1 KALE Mulungu analankhula ndi makolo mwa aneneri m'manenedwe ambiri ndi mosiyana-siyana,
2 koma pakutha pace pa masiku ano analankhula ndi ife ndi Mwana amene anamuika wolowa nyumba wa zonse, mwa Iyenso analenga maiko ndi am'mwamba omwe;
3 ameneyo, pokhala ali cinyezimiro ca ulemerero wace, ndi cizindikilo ceni ceni ca cikhalidwe cace, nanyamula zonse ndi mau a mphamvu yace, m'mene adacita ciyeretso ca zoipa, anakhala pa dzanja lamanja la Ukulu m'Mwamba,
4 atakhala wakuposa angelo, monga momwe adalowa dzina lakuposa iwo.
5 Pakuti kwa mngelo uti anati nthawi iri yonse, Iwe ndiwe Mwana wanga, Lero ine ndakubala Iwe? ndiponso, Ine ndidzakhala kwa iye Atate, Ndipo iye adzakhala kwa ine Mwana?
6 Ndipo pamene atenganso wobadwa woyamba kulowa naye m'dziko, anena, Ndipo amgwadire iye angelo onse a Mulungu.
7 Ndipo za angelo anenadi, Amene ayesa angelo ace mizimu, Ndi omtumikira iye akhale lawi lamoto;
8 Koma ponena za Mwana, ati, Mpando wacifumu wanu, Mulungu, ufikira nthawi za nthawi; Ndipo ndodo yacifumu yoongoka ndiyo ndodo ya ufumu wanu.
9 Mwakonda cilungamo, ndi kudana naco coipa; Mwa ici Mulungu, ndiye Mulungu wanu, wakudzozani Ndi mafuta a cikondwerero ceni ceni koposa anzanu.
10 Ndipo, Inu, Ambuye, paciyambipo munaika maziko ace a dziko, Ndipo miyamba iri nchito ya manja anu;
11 Iyo idzatayika; komatu mukhalitsa; Ndipo iyo yonse idzasuka mongamaraya;
12 Ndi monga copfunda mudzaipinda Monga maraya, ndipo idzasanduka; Koma Inu ndinu yemweyo, Ndipo zaka zanu sizidzatha.
13 Koma za mngelo uti anati nthawi iri yonse, Khala pa dzanja lamanja langa, Kufikira ndikaika adani ako mpando wa ku mapazi ako?
14 Kodi siiri yonse mizimu yotumikira, yotumidwa kuti itumikire iwo amene adzalowa cipulumutso?
1 Mwa ici tiyenera kusamaliradi zimene tidazimvazi kuti kapena tingatengedwe ndi kusiyana nazo.
2 Pakuti ngati mau adalankhulidwa ndi angelo adakhala okhazikika, ndipo colakwira ciri conse ndi cosamvera calandira mphotho yobwezera yolungama,
3 tidzapulumuka bwanji ife, tikapanda kusamala cipulumutso cacikuru cotero? cimene Ambuye adayamba kucilankhula, ndipo iwo adacimva anatilimbikitsira ife;
4 pocita umboni pamodzi nao Mulungunso ndi zizindikilo, ndi zozizwitsa ndi mphamvu za mitundu mitundu ndi zogawira za Mzimu Woyera, monga mwa cifuniro cace.
5 Pakuti sanagoniersera angelo dziko lirinkudza limene tinenali.
6 Koma wina anacita umboni pena, nati, Munthu nciani kuti mumkumbukila iye? Kapena mwana wa munthu kuti muceza naye?
7 Munamcepsa pang'ono ndi angelo, Mudambveka iye korona wa ulemerero ndi ulemu, Ndipo mudamuika iye wovang'anira nchito za manja anu;
8 Mudagonjetsa zonse pansi pa mapaziace. Pakuti muja adagonietsa zonse kwa iye, sanasiyapo kanthu kosamgoniera iye. Koma sitinayamba tsopano apa kuona zonse zimgonjera.
9 Koma timpenya iye amene adamcepsa pang'ono ndi angelo, ndiye Yesu, cifukwa ca zowawa za imfa, wobvala korona wa ulemerero ndi ulemu, kuti ndi cisomo ca Mulungu alawe imfa m'malo mwa munthu ali yense.
10 Pakuti kunamuyenera iye amene zonse ziri cifukwa ca iye, ndi zonse mwa Iye, pakutenga ana ambiri alowe ulemerero, kumkonza wamphumphu mtsogoleri woyamba wa cipulumutso cao mwa zowawa.
11 Pakuti iye wakuyeretsa ndi iwo akuyeretsedwa acokera onse mwa mmodzi; cifukwa ca ici alibe manyazi kuwacha iwo abale,
12 ndi kuti, ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga, Pakati pa Mpingo ndidzakuyimbirani.
13 Ndiponso, Ndidzamtama Iye. Ndiponso, Taonani, Ine ndi ana amene Mulungu anandipatsa,
14 Popeza tsono ana ndiwo a mwazi ndi nyama, Iyenso momwemo adalawa nao makhalidwe omwewo kuti mwa imfa akamuononge iye amene anali nayo mphamvu ya imfa, ndiye mdierekezi;
15 nakamasule iwo onse amene, cifukwa ca kuopa imfa, m'moyo wao wonse adamangidwa ukapolo.
16 Pakuti ndithu salandira angelo, koma alandira mbeu ya Abrahamu.
17 Potero kudamuyenera kufanizidwa ndi abale m'zonse, kuti akadzakhala mkulu wa ansembe wadfundo ndi wokhulupirika m'zinthu zakwa Mulungu, kuti apereke dipo la zoipa za anthu.
18 Pakuti popeza adamva zowawa, poyesedwa yekha, akhoza kuthandiza iwo amene ayesedwa.
1 Potero, abale oyera mtima, olandirana nao maitanidwe akumwamba, lingirirani za Mtumwi ndi. Mkuluwansembe wa cibvomerezo cathu, Yesu;
2 amene anakhala wokhulupirika kwa iye adamuikayo, monganso Mose m'nyumba yace yonse.
3 Pakuti ameneyo wayesedwa woyenera ulemerero woposa Mose, monga momwe iye amene anaimanga nyumba ali nao ulemerero woposa nyumbayi.
4 Pakuti nyumba iri yonse iri naye wina woimanga; koma wozimanga zonse ndiye Mulungu.
5 Ndipo Mosetu anali wokhulupirika m'nyumba yace yonse, monga mnyamata, acitire umboni izi zidzalankhulidwazi;
6 koma Kristu monga mwana, wosunga nyumba yace; ndife nyumba yace, ngati tigwiritsa kulimbika mtima ndi kudzitamandira kwa ciye-I mbekezoeo, kucigwira kufikira citsiriziro.
7 Momwemo, monga anena Mzimu Woyera, Lero ngati mudzamva mau ace,
8 Musaumitse mitima yanu, monga m'kupsetsa mtimamo, Monga muja tsiku la ciyesero m'cipululu,
9 Cimene makolo anu anandiyesa naco, Ndi kundibvomereza, Naona nchito zanga zaka makumi anai.
10 Momwemo ndinakwiya nao mbadwouwu, Ndipo ndinati, Nthawi zonse amasocera mumtima; Koma sanazindikira njira zangaiwowa;
11 Monga ndinalumbira m'ukali wanga: Ngati adzalowa mpumulo wanga!
12 Tapenyani, abale, kuti kapena ukakhale mwa wina wa inu mtima woipa wosakhulupira, wakulekana ndi Mulungu wamoyo;
13 komatu dandauliranani nokha tsiku ndi tsiku, pamene paehedwa, Lero; kuti angaumitsidwe wina wa inu ndi cenjerero la ucimo;
14 pakuti takhala ife olandirana ndi Kristu, ngatitu tigwiritsa ciyambi ca kutama kwathu kucigwira kufikira citsiriziro;
15 umo anenamo, Lero ngati mudzamva mau ace, Musaumitse mitima yanu, monga pa kupsetsa mtima.
16 Pakuti ndi ayani, pakumva, anapsetsa mtima? Kodi si onse aja adaturuka m'Aigupto ndi Mose?
17 Koma anakwiya ndi ayani zaka makumi anai? Kodi si ndi awo adacimwawo, amene matupi ao adagwa m'cipululu?
18 Ndipo adawalumbirira ayani kuti asalowe mpumulo wace?
19 Si awo kodiosamverawo? Ndipo tiona kuti sanakhoza kulowa cifukwa ca kusakhulupirira.
1 Cifukwa cace tiope kuti kapena likatsala lonjezano lakulowa mpumulo wace, wina wa inu angaoneke ngati adaliperewera.
2 Pakuti kwa ifenso walalikidwa Uthenga Wabwino, monganso kwa iwo; koma iwowa sanapindula nao mau omvekawo, popeza sanasanganizika ndi cikhulupiriro mwa iwo amene adawamva.
3 Popeza ife amene takhulupira tilowa mpumulowo, monga momwe ananena, Monga ndalumbira mu mkwiyowanga, Ngati adzalowa mpumulo wanga: zingakhale nebitozo zidatsirizika kuyambira kuzika kwa dziko lapansi.
4 Pakuti wanena pena za tsiku lacisanu ndi ciwiri, natero, Ndipo Mulungu anapumula tsiku lacisanu ndi ciwiri, kuleka nchito zace zonse
5 Ndipo m'menemonso, Ngati adzalowa mpumulo wanga.
6 Popeza tsono patsala kuti ena akalowa momwemo, ndi iwo amene Uthenga Wabwino unalalikidwa kwa iwo kale sanalowamo cifukwa ca kusamvera,
7 alangizanso tsiku lina, ndi kunena m'Davide, itapita nthawi yaikuru yakuti, Lero, monga kwanenedwakale, Lero ngati mudzamva mau ace, Musaumitse mitima yanu.
8 Pakuti ngati Yoswa akadawapumitsa iwo, sakadalankhuia m'tsogolomo za tsiku lina.
9 Momwemo utsalira mpumulo wa Sabata wa kwa anthu a Mulungu.
10 Pakuti iye amene adalowa mpumulo wace, adapumulanso mwini wace ku nchito zace, monganso Mulungu ku zace za iye.
11 Cifukwa cace ticite cangu ca kulowa mpumulowo, kuti f winaangagwe m'citsanzo comwe ca kusamvera.
12 Pakuti mau a Mulungu ali amoyo, ndi ocitacita, ndi akuthwa koposa lupanga lakuthwa konse konse, napyoza kufikira kugawira moyo ndi mzimu, ndi zimfundo ndi mafuta a m'mafupa, nazindikiritsa zolingirira ndi zitsimikizo za mtima.
13 Ndipo palibe colengedwa cosaonekera pamaso pace, koma zonse zikhala za pambalambanda ndi zobvundukuka pamaso pace pa iye amene ticita naye.
14 Popeza tsono tiri naye Mkuluwansembe wamkuru, wopyoza miyamba, Yesu Mwana wa Mulungu, tigwiritsitse cibvomerezo cathu.
15 Pakuti sitiri naye mkulu wa ansembe wosatha kumva cifundo ndi zofoka zathu; koma wayesedwa m'zonse monga momwe ife, koma wopanda ucimo.
16 Potero tilimbike mtima poyandikira mpando wacifumu wacisomo, kuti tilandire cifundo ndi kupeza cisomo ca kutithandiza nthawi yakusowa.
1 Pakuti mkulu wa ansembe ali yense, wotengedwa mwa anthu, amaikika cifukwa ca anthu m'zinthu za kwa Mulungu, kuti apereke mitulo, ndiponso nsembe, cifukwa ca macimo:
2 akhale wokhoza kumva cifundo ndi osadziwa ndi olakwa, popeza iye yekhanso amazingwa ndi cifoko;
3 ndipo cifukwa caceco ayenera, monga m'malo a anthuwo, moteronso m'malo a iye yekha, kupereka nsembe cifukwa ca macimo.
4 Ndipo palibe munthu adzitengera ulemuwo mwini wace, komatu iye amene aitanidwa ndi Mulungu, monga momwenso Aroni.
5 Koteronso Kristu sanadzilemekeza yekha ayesedwe Mkuluwansembe, komatu iye amene analankhula kwa iye, Mwana wanga ndi Iwe, Lero Ine ndakubala Iwe;
6 Monga anenanso mwina, Iwe ndiwe wansembe wa nthawizonse Monga mwa dongosolo la Melikizedeke.
7 Ameneyo, m'masiku a thupi lace anapereka mapemphero ndi mapembedzero pamodzi ndi kulira kwakukuru ndi misozi kwa iye amene anakhoza kumpulumutsa iye muimfa, ndipo anamveka popeza anaopa Mulungu,
8 angakhale anali Mwana, anaphunzira kumvera ndi izi adamva kuwawa nazo;
9 ndipo pamene anakonzeka wamphumphu anakhala kwa onse akumvera iye cifukwa ca cipulumutso cosatha;
10 wochedwa ndi Mulungu mkulu wa ansembe monga mwa dongosolo la Melikizedeke.
11 Za iye tirinao mau ambiri kuwanena, ndiotilaka powatanthauzira, popeza mwagontha m'makutu.
12 Pakuti mungakhale mwayenera kukhala aphunzitsi cifukwa ca nyengoyi, muli nako kusowanso kuti wina aphunzitse inu zoyamba za ciyambidwe ca maneno a Mulungu; ndipo mukhala onga ofuna mkaka, osati cakudya cotafuna.
13 Pakuti yense wakudya mkaka alibe cizolowezi ca mau a cilungamo; pakuti ali khanda.
14 Koma cakudya cotafuna ciri ca anthu akulu misinkhu, amene mwa kucita nazo anazoloweretsa zizindikiritso zao kusiyanitsa cabwino ndi coipa.
1 Mwa ici, polekana nao mau a ciyambidwe ca Kristu, tipitirire kutsata ukulu msinkhu; osaikanso maziko a kutembenuka mtima kusiyana nazo nchito zakufa, ndi a cikhulupiriro ca pa Mulungu,
2 a ciphunzitso ca ubatizo, a kuika manja, a kuuka kwa akufa, ndi a ciweruziro cosatha.
3 Ndipo ici tidzacita, akatilola Mulungu.
4 Pakuti sikutheka kuwakonzanso, atembenuke mtima, iwo amene anaunikidwa pa nthawi yace, nalawa mphatso ya Kumwamba, nakhala olandirana naye Mzimu Woyera,
5 nalawa mau okoma a Mulungu, ndi mphamvu ya nthawi irinkudza,
6 koma anagwa m'cisokero; popeza adzipaeikiranso okha Mwana wa Mulungu, namcititsa manyazi poyera.
7 Pakuti nthaka imene idamwa mvula iigwera kawiri kawiri, nipatsa therere loyenera iwo amene adailimira, ilandira dalitso locokera kwa Mulungu:
8 koma ikabala minga ndi mitungwi, itayika; nitsala pang'ono ikadatembereredwa; citsiriziro cace ndico kutenthedwa.
9 Koma, okondedwa, takopeka mtima kuti za inu ziri zoposa ndi zophatikana cipulumutso, tingakhale titero pakulankhula;
10 pakuti Mulungu sali wosalungama kuti adzaiwala nchito yanu, ndi cikondico mudacionetsera ku dzina lace, umo mudatumikira oyera mtima ndi kuwatumikirabe.
11 Koma tikhumba kuti yense wa inu aonetsere cangu comweci colinga ku ciyembekezo cokwanira kufikira citsiriziro;
12 kuti musakhale aulesi, koma akuwatsanza iwo amene alikulowa malonjezano mwa cikhulupiriro ndi kuleza mtima.
13 Pakuti pamene Mulungu analonjezana naye Abrahamu, popeza analibe wamkuru woposa kumlumbira, analumbira pa iye yekha,
14 nati, Kudalitsatu ndidzakudalitsa iwe, ndipo kucurukitsa ndidzakucurukitsa iwe.
15 Ndipo potero atapirira analandira lonjezanolo.
16 Pakuti anthu amalumbira pa wamkulu; ndipo m'citsutsano cao ciri conse lumbiro litsiriza kutsimikiza.
17 Momwemo Mulungu, pofuna kuonetsera mocurukira kwa olowa a lonjezano kuti cifuniro cace sicisinthika, analowa pakati ndi lumbiro;
18 kuti mwa zinthu ziwiri zosasinthika, m'mene Mulungu sakhoza kunama, tikakhale naco coticenjeza colimba, ife amene tidathawira kucigwira ciyembekezo coikika pamaso pathu;
19 cimene tiri naco ngati nangula wa moyo, cokhazikika ndi colimbanso, ndi cakulowa m'katikati mwa cophimba;
20 m'mene Yesu mtsogoleri analowamo cifukwa ca ife, atakhala mkulu wa ansembe nthawi yosatha monga mwa dongosolo la Melikizedeke.
1 Pakuti Melikizedeke uyu, Mfumu ya Salemu, wansembe wa Mulungu Wamkulukulu, amene anakomana ndi Abrahamu, pobwera iye adawapha mafumu aja, namdalitsa,
2 amenenso Abrahamu anamgawira limodzi la magawo khumi la zonse (ndiye posandulika, poyamba ali Mfumu ya cilungamo, pameneponso Mfumu ya Salemu, ndiko, Mfumu ya mtendere;
3 wopanda atate wace, wopanda amace, wopanda mawerengedwe a cibadwidwe cace, alibe ciyambi ca masiku ace kapena citsiriziro ca moyo wace, wofanizidwa ndi Mwana wa Mulungu), iyeyu wakhala wansembe kosalekeza.
4 Koma tapenyani ukulu wace wa iyeyu, amene Abrahamu, kholo lalikuru, anampatsa limodzi la magawo khumi la zosankhika za kunkhondo.
5 Ndipo iwotu mwa ana a Levi akulandira nchito yakupereka nsembe, ali nalo lamulo lakuti atenge limodzi la magawo khumi kwa anthu monga mwa cilamulo, ndiko kwa abaleao, angakhale adaturuka m'cuuno ca Abrahamu;
6 koma iye amene mawerengedwe a cibadwidwe cace sacokera mwa iwo, anatenga limodzi la magawo khumi kwa Abrahamu, namdalitsa iye amene ali nao malonjezano.
7 Ndipo popanda citsutsano konse wamng'ono adalitsidwa ndi wamkuru.
8 Ndipo pano anthu ofeka alandira limodzi la magawo khumi; koma apo iye, woti adamcitira umboni kuti ali ndi moyo.
9 Ndipo kuli ngati kunena, mwa Abrahamu Levinso wakulandira limodzi limodzi la magawo khumi adapereka limodzi la magawo khumi;
10 pakuti pajapo anali m'cuuno ca atate wace, pamene Melikizedeke anakomana naye.
11 Ndipo pakadakhala ungwiro mwa unsembe wa Cilevi (pakuti momwemo anthu analandira cilamulo), pakadatsala kusowa kotani kuti auke wansembe wina monga mwa dongosolo la Melikizedeke, wosayesedwa monga mwa dongosolo la Aroni?
12 Pakuti posandulika unsembe, kufunikanso kuti lamulo lisandulike.
13 Pakuti iye amene izi zineneka za iye, akhala wa pfuko lina, wa ili palibe munthu watumikira guwa la nsembe.
14 Pakuti kwadziwikadi kuti Ambuye wathu anaturuka mwa Yuda; za pfuko ili Mose sanalankhula kanthu ka ansembe.
15 Ndipo kwadziwikatu koposa ndithu, ngati auka wansembe wina monga mwa mafanidwe a Melikizedeke,
16 amene wakhala si monga mwa lamulo la lamuliro la kwa thupi, komatu monga mwa mphamvu ya moyo wosaonongeka;
17 pakuti amcitira umboni, Iwe ndiwe wansembe nthawi yosatha Monga mwa dongosolo la Melikizedeke.
18 Pakutitu kuli kutaya kwace kwa lamulo lidadza kalelo, cifukwa ca kufoka kwace, ndi kusapindulitsa kwace,
19 (pakuti cilamulo sicinacitira kanthu kakhale kopanda cirema), ndipo kulinso kulowa naco ciyembekezo coposa, cimene tiyandikira naco kwa Mulungu.
20 Ndipo monga momwe sikudacitika kopanda lumbiro;
21 (pakuti iwotu anayesedwa ansembe kopanda lumbiro; koma iye ndi lumbiro mwa iye emeoe ananena kwa iye, Walumbira Ambuye ndipo sadzalapa, Iwe ndiwe wansembe nthawi yosatha).
22 Momwemonso Yesu wakhala Nkhoswe ya pangano loposa.
23 Ndipo iwo ndiwo ambiri anakhala ansembe, popeza imfa idawaletsa asakhalebe;
24 koma iye cifukwa kuti akhala iye nthawi yosatha ali nao unsembe wosasinthika,
25 kucokera komwekoakhoza kupulumutsa konse konse iwo akuyandikira kwa Mulungu mwa iye, popeza ali nao moyo wace cikhalire wa kuwapembedzera iwo.
26 Pakuti mkulu wa ansembe wotere anatiyenera ife, woyera mtima, wopanda coipa, wosadetsedwa, wosiyana ndi ocimwa, wakukhala wopitirira miyamba;
27 amene alibe cifukwa ca kupereka nsembe tsiku ndi tsiku monga akulu a ansembe, yoyambira cifukwa ca zoipa za iwo eni, yinayi cifukwa ca zoipa za anthu; pakuti ici anacita kamodzi, kwatha, podzipereka yekha.
28 Pakuti cilamulo cimaika akuru a ansembe anthu, okhala naco cifoko; koma mau a lumbirolo, amene anafika citapita cilamulo, aika Mwana, woyesedwa wopanda cirema ku nthawi zonse.
1 Koma mutu wafzi tanenazi ndi uwu: Tiri naye Mkuruwansembe wotere, amene anakhala pa dzanja lamanja la mpando wacifumu wa Ukulu m'Kumwamba,
2 Mtumiki wa malo opatulika, ndi wa cihema coona, cimene Ambuye anacimanga, si munthu ai.
3 Pakuti mkulu wa ansembe ali yense aikidwa kupereka mitulo, ndiponso nsembe; potero nkufunika kuti ameneyo akhale nako kanthunso kakupereka,
4 Ndipo iye akadakhala padziko, sakadakhala konse wansembe, popeza pali iwo akupereka mitulo monga mwa lamulo;
5 amene atumikira cifaniziro ndi mthunzi wa zakumwambazo monga Mose acenjezedwa m'mene anafuna kupanga cihema: pakuti, Cenjera, ati, ucite zonse monga mwa citsanzoco caonetsedwa kwa iwe m'phiri.
6 Koma tsopano iye walandira citumikiro comveka coposa, umonso ali Nkhoswe ya pangano labwino loposa, limene likhazikika pa malonjezano oposa.
7 Pakuti loyamba lija likadakhala lopanda cirema sakadafuna malo a laciwirilo.
8 Pakuti powachulira iwo cifukwa, anena, Taonani, akudza masiku, anena Ambuye, Ndipo ndidzapangana pangano latsopano ndi nyumba ya Israyeli, ndi nyumba ya Yuda,
9 Losati longa pangano ndinalicita ndi makolo ao, Tsikuli ndinawagwira kudzanja iwo kuwatsogolera aturuke m'dziko la Aigupto; Kuti iwo sanakhalabe m'pangano langa, Ndipo loe sindinawasamalira iwo, anena Ambuye,
10 Pakuti ili ndi pangano ndidzalipangana ndi nyumba ya Israyeli, Atapita masiku ajawa, anena Ambuye: Ndidzapatsa malamulo anga kuwalonga m'nzeru zao, Ndipo pamtima pao ndidzawalemba iwo; Ndipo ndidzawakhalira iwo Mulungu, Ndipo iwo adzandikhalira Ine anthu:
11 Ndipo sadzaphunzitsa yense mfulu mnzace, Ndipo yense mbale wace, ndi kuti, Zindikira Ambuye: Pakuti onse adzadziwa Ine, Kuyambira wamng'ono kufikira wamkuru wa iwo.
12 Kuti ndidzacitira cifundo rosalungama zao, Ndipo zoipa zao sindidzazikumbukanso.
13 Pakunena iye, Latsopano, anagugitsa loyambali. Koma cimene cirimkuguga ndi kusukuluka, cayandikira kukanganuka.
1 Ndipo cingakhale cipangano coyambaci cinali nazo zoikika za kulambira, ndi malo opatulika a pa dziko lapansi.
2 Pakuti cihema cidakonzeka, coyamba cija, m'menemo munali coikapo nyali, ndi gome, ndi mkate woonekera; paja paitanidwa Malo Opatulika,
3 Koma m'kati mwa cophimba caciwiri, cihema conenedwa Malo Opatulikitsa;
4 okhala nayo mbale ya zofukiza yagolidi ndi likasa la cipangano, lokuta ponsepo ndi golidi, momwemo munali mbiya yagolidi yosungamo mana, ndi ndodo ya Aroni idapukayo, ndi magome a cipangano;
5 ndi pamwamba pace akerubi a ulemerero akucititsa mthunzi pacotetezerapo; za izi sitikhoza kunena tsopano padera padera.
6 Ndipo izi zitakonzeka kotero, ansembe amalowa m'cihema coyamba kosalekeza, ndi kutsiriza kulambirako;
7 koma kulowa m'caciwiri, mkuru wa ansembe yekha kamodzi pacaka, wosati wopanda mwazi, umene apereka cifukwa ca iye yekha, ndi zolakwa za anthu;
8 Mzimu Woyera wodziwitsa nako, kuti njira yolowa nayo ku malo opatulika siinaonetsedwe, pokhala cihema coyamba ciri ciriri;
9 ndico ciphiphiritso ca ku nthawi yomweyi, m'mene mitulo ndi nsembenso zinaperekedwa zosakhoza, ponena za cikumbu mtima, kuyesa wangwiro wolambirayo.
10 Popeza akhala zoikika za thupi zokha (ndi zakudya, ndi zakumwa, ndi masambidwe osiyana-siyana), oikidwa kufikira nthawi yakukonzanso.
11 Koma atafika Kristu, Mkuluwansembe wa zokoma zirinkudza, mwa cihema cacikuru ndi cangwiro coposa, cosamangika ndi manja, ndiko kunena kuti, cosati ca ciiengedweici,
12 kapena mwa mwazi wa mbuzi ndi ana a ng'ombe, koma mwa mwazi wa iye yekha, analowa kamodzi ku malo opatulika, atalandirapo ciombolo cosatha.
13 Pakuti ngati mwazi wa mbuzi ndi ng'ombe zamphongo, ndi makala a ng'ombe yamthandi owazawaza pa iwo odetsedwa, upatutsa kufikira ciyeretso ca thupi;
14 koposa kotani nanga mwazi wa Kristu amene anadzipereka yekha wopanda cirema kwa Mulungu mwa Mzimu wosatha, udzayeretsa cikumbu mtima canu kucisiyanitsa ndi nchito zakufa, kukatumikira Mulungu wamoyo?
15 Ndipo mwa ici ali Nkhoswe ya cipangano catsopano, kotero kuti, popeza kudacitika imfa yakuombola zolakwa za pa cipangano coyamba, oitanidwawo akalandire lonjezano la zolowa zosatha.
16 Pakuti pamene pali copangiratu pafunika pafike imfa ya wolemberayo.
17 Pakuti copangiratu ciona mphamvu atafa mwini wace; popeza ciribe mphamvu konse pokhala wolemberayo ali ndi moyo;
18 momwemo coyambaconso sicinakonzeka copanda mwazi.
19 Pakuti pamene Mose adalankhulira anthu once lamulo liri lonse monga mwa cilamulo, anatenga mwazi wa ana a ng'ombe ndi mbuzi, pamodzi ndi madzi ndi ubweya wofiira ndi hisope, nawaza buku lomwe, ndi anthu onse,
20 nati, 1 Uwu ndi mwazi wa cipangano Mulungu adakulamulirani.
21 Ndiponso cihema ndi zotengera zonse za utumikiro anaziwaza momwemo ndi mwaziwo.
22 Ndipo monga mwa cilamulo zitsala zinthu pang'ono zosayeretsedwa ndi mwazi, ndipo 2 wopanda kukhetsa mwazi kulibe kumasuka.
23 Pomwepo padafunika kuti 3 zifaniziro za zinthu za m'Mwamba ziyeretsedwe ndi izi; koma zam'mwamba zeni zeni ziyeretsedwe ndi nsembe zoposa izi.
24 Pakuti 4 Kristu sanalowa m'malo opatulika omangika ndi manja, akutsanza oonawo; komatu m'Mwamba momwe, 5 kuonekera tsopano pamaso pa Mulungu cifukwa ca ife;
25 kosati kuti adzipereke yekha kawiri kawiri; 6 monga mkulu wa ansembe alowa m'malo opatulika caka ndi caka ndi mwazi wosati wace;
26 cikadatero, kukadamuyenera kumva zowawa kawiri kawiri kuyambira kuzika kwa dziko lapansi; kama tsopano 7 kamodzi pa citsirizo ca nthawizo waonekera kucotsa ucimo mwa nsembe ya iye yekha.
27 Ndipo popeza 8 kwaikikatu kwa anthu kufa kamodzi, ndipo 9 atafa, ciweruziro;
28 kotero 10 Kristunso ataperekedwa nsembe kamodzi kukasenza macimo a ambiri, 11 adzaonekera pa nthawi yaciwiri, wopanda ucimo, kwa iwo amene amlindirira, kufikira cipulumutso.
1 mthunzi wa zokoma zirinkudza, osati cifaniziro ceni ceni ca zinthuzo, sicikhozatu, ndi nsembe zomwezi caka ndi caka, zimene azipereka kosalekeza, kuwayesera angwiro iwo akuyandikira.
2 Pakadapanda kutero, kodi sakadaleka kuzipereka, cifukwa otumikirawo sakadakhala naco cikumbu mtima ca macimo, popeza adayeretsedwa kamodzi?
3 Komatu mu izizo muli cikumbukiro ca macimo caka ndi caka.
4 Pakuti sikutheka kuti mwazi wa ng'ombe zamphongo, ndimbuzi ukacotsera macimo.
5 Mwa ici polowa m'dziko lapansi, anena, Nsembe ndi copereka simunazifuna, Koma thupi munandikonzera Ine.
6 Nsembe zopsereza zamphumphu ndi za kwa macimo simunakondwera nazo;
7 Pamenepo ndinati, Taonani, ndafika, (Pamutu pace pa buku palembedwa za Ine) Kudzacita cifuniro canu, Mulungu,
8 Pakunena pamwamba apa, kuti, Nsembe ndi zopereka ndi nsembe zopsereza zamphumphu ndi za kwa macimo simunazifuna, kapena kukondwera nazo (zimene ziperekedwa monga mwa lamulo),
9 pamenepo anati, Taonani, ndafika kudzacita cifuniro canu. Acotsa coyambaco, kuti akaike caciwirico.
10 Ndi cifuniro cimeneco tayeretsedwa mwa copereka ca thupi la Yesu Kristu, kamodzi, kwatha.
11 Ndipotu wansembe ali yenseamaima tsiku ndi tsiku, natumikira, napereka nsembe zomwezi kawiri kawiri, zimene sizikhoza konse kucotsa macimo;
12 koma iye, m'mene adapereka nsembe imodzi cifukwa ca macimo, anakhala pa dzanja lamanja la Mulungu cikhalire;
13 kuyambira pomwepo alindirira, kufikira adani ace aikidwa akhale mpando ku mapazi ace.
14 Pakuti ndi cipereko cimodzi anawayesera angwiro cikhalire iwo oyeretsedwa.
15 Koma Mzimu Woyeranso aticitira umboni; pakuti adatha kunena,
16 ici ndi cipangano ndidzapangana nao, Atapira masiku ajawo, anena Ambuye: Ndidzapereka malamulo anga akhale pamtima pao; Ndipo pa nzeru zao ndidzawalemba;
17 Ndipo macimo ao ndi masayeruziko ao sindidzawakumbukilanso.
18 Koma pomwe pali cikhululukiro ca macimo palibenso copereka ca kwaucimo.
19 Ndipo pokhala naco, abale, cilimbikitso cakulowa m'malo opatulika, ndi mwazi wa Yesu,
20 pa njira yatsopano ndi yamoyo, imene adatikonzera, mwa cocinga, ndico thupi lace;
21 ndipo popeza tiri naye wansembe wamkuru wosunga nyumba ya Mulungu;
22 tiyandikire ndi mtima woona, m'cikhulupiriro cokwanira, ndi mitima yathu yowazidwa kuicotsera cikumbu mtima coipa, ndi matupi athu osambitsidwa ndi madzi oyera;
23 tigwiritse cibvomerezo cosagwedera ca ciyembekezo cathu, pakuti wolonjezayo ali wokhulupirika;
24 ndipo tiganizirane wina ndi mnzace kuti tifulumizane ku cikondano ndi nchito zabwino,
25 osaieka kusonkhana kwathu pamodzi, monga amacita ena, komatu tidandaulirane, ndiko koposa monga momwe muona tsiku lirikuyandika.
26 Pakuti tikacimwa ife eni ace, titatha kulandira cidziwitso ca coonadi, siitsalanso nsembe ya kwa macimo,
27 koma kulindira kwina koopsa kwa ciweruziro, ndi kutentha kwace kwa mota wakuononga otsutsana nao.
28 Munthu wopeputsa cilamulo ca Mose angofa opanda cifundo pa mboni ziwiri kapena zitatu:
29 ndipo mutani, kulanga koposa kotani nanga adzayesedwa woyenera iye amene anapondereza Mwana wa Mulungu, nayesa mwazi wa cipangano umene anayeretsedwa nao cinthu wamba, z nacitira cipongwe Mzimu wa cisomo;
30 pakuti timdziwa iye amene anati, 1 Kubwezera cilango nkwanga, loe ndidzabwezera. Ndiponso; 2 Ambuye adzaweruza anthu ace.
31 3 Kugwa m'manja a Mulungu wamoyo nkoopsa.
32 Koma tadzikumbursani masiku akale, m'menemo mutaunikidwa 4 mudapirira citsutsano cacikuru ca zowawa;
33 pena pocitidwa 5 cinthu cooneredwa mwa matonzo ndi zisautso; penanso polawana nao iwo ocitidwa zotere.
34 Pakuti 6 munamva cifundo ndi iwo a m'ndende, ndiponso mudalola mokondwera kulandidwa kwa cuma canu, 7 pozindikira kuti muli naco nokha cuma coposa caeikhalire.
35 Potero musataye kulimbika kwanu, kumene kuli naco cobwezera mphotho cacikuru.
36 Pakuti cikusowani cipiriro, kuti 8 pamene mwacita cifuniro ca Mulungu, mukalandire lonjezano.
37 9 Pakuti katsala kanthawi kakang'onong'ono, Ndipowakudzayoadzafika, wesacedwa.
38 10 Koma wolungama wangayo adzakhala ndi moyo wocokera m'cikhulupiriro: Ndipo ngati abwerera, moyo wanga ulibe kukondwera mwaiye.
39 Koma ife si ndife 11 a iwo akubwerera kulowa citayiko; koma 12 a iwo a cikhulupiriro ca ku cipulumutso ca moyo.
1 Koma cikhulupiriro ndico cikhazikitso ca zinthu zoyembekezeka, ciyesero ca zinthu zosapenyeka.
2 Pakuti momwemo akulu anacitidwa umboru.
3 Ndi cikhulupiriro tizindikira kuti maiko ndi a m'mwamba omwe anakonzedwa ndi mau a Mulungu, kotero kuti zinthu zopenyeka sizinapangidwa zocokera mwa zoonekazo.
4 Ndi cikhulupiriro Abeli anapereka kwa Mulungu nsembe yoposa ija ya Kami, mene anacitidwa umboni nayo kuti anali wolungama; nacitapo umboni Mulungu pa mitulo yace; ndipo momwemo iye, angakhale adafa alankhulabe.
5 Ndi cikhulupiriro Enoke anatengedwa kuti angaone imfa; ndipo sanapezeka, popeza Mulungu adamtenga: pakuti asanamtenge, anacitidwa umboni kuti anakondweretsa Mulungu;
6 koma wopanda cikhulupiriro sikutheka kumkondweretsa; pakuti iye wakudza kwa Mulungu ayenera kukhulupirira kuti alipo, ndi kuti ali wobwezera mphotho iwo akumfuna iye.
7 Ndi cikhulupiriro Nowa, pocenjezedwa ndi Mulungu za zinthu zisanapenyeke, ndi pocita mantha, anamanga cingalawa ca kupulumutsiramo iwo a m'nyumba yace; kumene anatsutsa nako dziko lapansi, nakhala wolowa nyumba wa cilungamo ciri monga mwa cikhulupiriro.
8 Ndi cikhulupiriro Abrahamu, poitanidwa, anamvera kuturuka kunka ku malo amene adzalandira ngati colowa; ndipo anaturuka wosadziwa kumene akamukako.
9 Ndi cikhulupiriro anakhala mlendo ku dziko la lonjezano, losati lace, nakhalira m'mahema pamodzi ndi Isake ndi Yakobo, olowa nyumba pamodzi ndi iye a lonjezano lomwelo;
10 pakuti analindirira mudzi wokhala nao maziko, mmisiri wace ndi womanga wace ndiye Mulungu.
11 Ndi cikhulupiriro Sara yemwe analandira mphamvu yakukhala ndi pakati, patapita nthawi yace, popeza anamwerengera wokhulupirika iye amene adalonjeza;
12 mwa icinso kudacokera kwa mmodzi, ndiye ngati wakufa, aunyinji ngati nyenyezi za m'mwamba, ndi ngati mcenga, uli m'mbali mwa nyanja, osawerengeka.
13 Iwo onse adamwalira m'cikhulupiriro, osalandira malonjezano, komatu adawaona ndi kuwalankhula kutali, nabvomereza kuti ali alendo ndi ogonera padziko.
14 Pakuti wo akunena zotere aonetserapo kuti alikufuna dziko likhale lao.
15 Ndipotu akadakumbukila lijalo adaturukamo akadaona njira yakubwera nayo.
16 Koma tsopano akhumba lina loposa, ndilo la m'Mwamba; mwa ici Mulungu sacita manyazi nao poitanidwa Mulungu wao; pakuti adawakonzera mudzi.
17 Ndi cikhulupiriro Abrahamu, poyesedwa, anapereka nsembe Isake, ndipo iye amene adalandira malonjezano anapereka mwana wace wayekha;
18 amene kudanenedwa za iye, kuti, Mwa Isake mbeu yako idzaitanidwa:
19 poyesera iye kuti Mulungu ngwokhoza kuukitsa, ngakhale kwa akufa; kucokera komwe, paciphiphiritso, anamlandiranso.
20 Ndi cikhulupiriro Isake anadalitsa Yakobo ndi Esau, zingakhale za zinthu zirinkudza,
21 Ndi cikhulupiriro Yakobo, poti alinkufa, anadalitsa yense wa ana a Yosefe; napembedza potsamira pa mutu wa ndodo yace.
22 Ndi cikhulupiriro, Yosefe, pakumwalira, anachula za maturukidwe a ana a Israyeli; nalamulira za mafupa ace.
23 Ndi cikhulupiriro Mose, pobadwa, anabisidwa miyezi itatu ndi akumbala, popeza anaona kuti ali mwana wokongola; ndipo sanaopa cilamuliro ca mfumu.
24 Ndi cikhulupiriro Mose, atakula msinkhu, anakana kuchedwa mwana wace wa mwana wamkazi wa Farao;
25 nasankhula kucitidwa zoipa pamodzi ndi anthu a Mulungu, kosati kukhala nazo zokondweretsa za zoipa nthawi;
26 nawerenga thonzo la Kristu cuma coposa zolemera za Aigupto; pakuti anapenyerera cobwezera ca mphotho.
27 Ndi cikhulupiriro anasiya Aigupto, wosaopa mkwiyo wa mfumu; pakuti anapirira molimbika monga ngari kuona wosaonekayo.
28 Ndi cikhulupiriro 1 anacita Paskha, ndi kuwaza kwa mwazi, kuti wakuononga ana oyamba angawakhudze iwo.
29 Ndi cikhulupiriro 2 anaoloka Nyanja Yofiira kupita ngati pamtunda: ndiko Aaigupto poyesanso anamizidwa.
30 Ndi cikhulupiriro 3 malinga a Yeriko adagwa atazunguliridwa masiku asanu ndi awiri.
31 Ndi cikhulupiriro 4 Rahabi wadama uja sanaonongeka pamodzi ndi osamverawo, popeza analandira ozonda ndi mtendere.
32 Ndipo ndinene cianinso? pakuti idzandiperewera nthawi ndifotokozere za 5 Gideoni, 6 Baraki, 7 Samsoni, 8 Yefita; za 9 Davide, ndi 10 Samueli ndi aneneri;
33 amene mwa cikhulupiriro anagonjetsa maufumu, anacita cilungamo, analandira malonjezano, 11 anatseka pakamwa mikango,
34 12 nazima mphamvu ya moto, 13 napulumuka lupanga lakuthwa, 14 analimbikitsidwa pokhala ofok a, anakula mphamvu kunkhondo, 15 anapitikitsa magulu a nkhondo yacilendo.
35 16 Akazi analandira akufa ao mwa kuuka kwa akufa; ndipo 17 ena anakwapulidwa, osalola kuomboledwa,
36 kuti akalandire kuuka koposa; koma ena anayesedwa ndi matonzo ndi zokwapulira, ndiponso nsinga, ndi 18 kuwatsekera m'ndende;
37 19 anaponyedwa miyala, anacekedwa pakati, anayesedwa, anaphedwa ndi lupanga, anayendayenda obvala zikopa zankhosa, ndi zikopa zambuzi, nakhala osowa, osautsidwa, ocitidwa zoipa,
38 (amenewo dziko lapansi silinayenera iwo), osokerera m'mapululu, ndi m'mapiri, ndi 20 m'mapanga, ndi m'mauna a dziko.
39 Ndipo iwo onse 21 adacitidwa umboni mwa cikhulupiriro, sanalandira lonjezanolo,
40 22 popeza Mulungu adatikonzera ife kanthu koposa, kuti iwo asayesedwe amphumphu opanda ife.
1 Cifukwa cace ifenso, popeza tizingidwa nao mtambo waukuru wotere wa mboni, titaye colemetsa ciri conse, ndi cimoli Iimangotizinga, ndipo tithamange mwacipiriro makaniwo adatiikira, ndi kupenyerera woyambira ndi womariza wa cikhulupiriro cathu,
2 Yesu, ameneyo, cifukwa ca cimwemwe coikidwaco pamaso pace, anapirira mtanda, nanyoza manyazi, nakhala pa dzanja lamanja la mpando wacifumu wa Mulungu,
3 Pakuti talingirirani iye amene adapirira ndi ocimwa otsutsana naye kotere, kuti mungaleme ndi kukomoka m'moyo mwanu.
4 Simunakana kufikira mwazi pogwirana nalo cimo;
5 ndipo mwaiwala dandauliro limene linena nanu monga ndi ana, Mwana wanga, usayese copepuka kulanga kwa Ambuye, Kapena usakomoke podzudzulidwa ndilye;
6 Pakuti iye amene Ambuye amkonda amlanga, Nakwapula mwana ali yense amlandira.
7 Mukapirira kufikira kulangidwa Mulungu acitira inu monga ngati ana; pakuti mwana wanji amene atate wace wosamlanga?
8 Koma ngati mukhala opanda cilango, cimene onse adalawako, pamenepo muli am'thengo, si ana ai.
9 Komanso, tinali nao atate a thupi lathu akutilanga, ndipo tinawalemekeza; kodi sitidzagonjera Atate wa mizimu koposa nanga, ndi kukhala ndi moyo?
10 Pakutitu iwo anatilanga masiku owerengeka monga kudawakomera; koma iye atero, kukatipindulitsa, kuti tikalandirane nao pa ciyero cace.
11 Chango ciri conse, pakucitika, sicimveka cokondwetsa, komatu cowawa; koma citatha, cipereka cipatso ca mtendere, kwa iwo ozoloweretsedwa naco, ndico ca cilungamo.
12 Mwa ici limbitsani manja ogooka, ndi maondo olobodoka;
13 ndipo lambulani miseu yolunjika yoyendamo mapazi anu, kuti cotsimphinaco cisapatulidwe m'njira, koma ciciritsidwe.
14 Londolani mtendere ndi anthu onse, ndi ciyeretso cimene, akapanda ici, palibe mmodzi adzaona Ambuye:
15 ndi kuyang'anira kuti pangakhale wina wakuperewera cisomo ca Mulungu, kuti ungapuke muzu wina wa kuwawa mtima ungabvute inu, ndipo aunyinji angadetsedwe nao;
16 kuti pangakhale wacigololo, kapena wamnyozo, ngati Esau, amene anagulitsa ukulu wace wobadwa nao mtanda umodzi wa cakudya.
17 Pakutf mudziwa kutinso pamene anafuna kulowa dalitsolo, anakanidwa (pakuti sanapeza malo akulapa), angakhale analifunafuna ndi misozi.
18 Pakuti simunayandikira phiri lokhudzika, ndi lakupsya moto, ndi pakuda bii, ndi mdima, ndi namondwe,
19 ndi mau a lipenga, ndi maaenedwe a mau, manenedweamene iwo adamvawo anapempha kuti asawaonjezerepo mau;
20 pakuti sanakhoza kulola colamulidwaco. Ingakhale nyama ikakhudza phirilo, idzaponyedwa miyala;
21 ndipo maonekedwewo anali oopsa otere, kuti Mose anati, Ndiopatu ndi kunthunthumira.
22 Komatu mwayandikira ku phiri la Ziyoni, ndi mudzi wa Mulungu wamoyo, Yerusalemu wa Kumwamba, ndi kwa unyinji wocuruka wa angelo,
23 ndi kwa msonkhano wa onse ndi Mpingo wa obadwa oyamba olembedwa m'Mwamba, ndi kwa Mulungu Woweruza wa onse, ndi kwa mizimu ya olungama oyesedwa angwiro,
24 ndi kwa Yesu Nkhoswe ya cipangano catsopano, ndi kwa mwazi wa kuwaza wakulankhula cokoma coposa mwazi wa Abeli.
25 Penyani musakane wolankhulayo. Pakuti ngati iwowa sanapulumuka, pomkana iye amene anawacenjeza padziko, koposatu sitidzapulumuka ife, odzipatulira kwa iye wa Kumwamba;
26 amene mau ace anagwedeza dziko pamenepo; koma tsopano adalonjeza, ndi kuti, Kamodzinso ndidzagwedeza, si dziko lokha, komanso m'mwamba.
27 Ndipo ici, cakuti kamodzinso, cilozera kusuntha kwace kwa zinthu zogwedezeka, monga kwa zinthu zolengedwa, kuti zinthu zosagwedezeka zikhale.
28 Mwa ici polandira ufumu wosagwedezeka, tikhale naco cisomo, cimene tikatumikire naco Mulungu momkondweretsa, ndi kumcitira ulemu ndi mantha.
29 Pakuti 1 Mulungu wathu ndiye mota wonyeketsa.
1 Cikondi ca pa abale cikhalebe.
2 Musaiwale kucereza alendo; pakuti mwa ici ena anacereza angelo osacidziwa.
3 Kumbukilani am'nsinga, monga am'nsinga anzao; ocitidwa zoipa, monga ngati inunso adatero nanu m'thupi.
4 Ukwati ucitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; pakuti adama ndi acigololo adzawaweruza Mulungu.
5 Mtima wanu ukhale wosakonda cuma; zimene muli nazo zikukwanireni; pakuti iye anati, Sindidzakusiya konse, kungakhale kukutaya, sindidzakutaya ndithu.
6 Kotero kuti tinena molimbika mtima, Mthandizi wanga ndiye Ambuye; smdidzaopa; Adzandicitira ciani munthu?
7 Kumbukilani atsogoleri anu, amene analankhula nanu Mau a Mulungu; ndipo poyang'anira citsiriziro ca mayendedwe ao mutsanze cikhulupiriro cao.
8 Yesu Kristu ali yemweyo dzulo, ndi lero, ndi ku nthawi zonse.
9 Musatengedwe ndi maphunzitso a mitundu mitundu, ndi acilendo; pakuti nkokoma kuti mtima ukhazikike ndi cisomo; kosati ndi zakudya, zimene iwo adazitsata sanapindula nazo.
10 Tiri nalo guwa la nsembe, limene iwo akutumikira cihema alibe ulamuliro wa kudyako.
11 Pakuti matupi a nyama zija, mwazi wa izo umatengedwa ndi mkulu wa ansembe kulowa m'malo opatulidwa, cifukwa ca zoipa, amatenthedwa kunja kwa tsasa.
12 Mwa ici Yesunso, kuti akayeretse anthuwo mwa mwazi wa iye yekha, adamva cowawa kunja kwa cipata.
13 Cifukwa cace titurukire kwa iye kunja kwa tsasa osenza thonzo lace.
14 Pakuti pano tiribe mudzi wokhalitsa, komatu tifunafuna ulinkudzawo.
15 Potero mwa iye tipereke ciperekere nsembe yakuyamika Mulungu, ndiyo cipatso ca milomo yobvomereza dzina lace.
16 Koma musaiwale kucitira cokoma ndi kugawira ena; pakuti nsembe zotere Mulunguakondweranazo.
17 Mverani atsogoleri anu, nimuwagonjere; pakuti alindirira moyo wanu, monga akuwerengera; kuti akacite ndi cimwemwe, osati mwacisoni: pakuti ici sicikupindulitsani inu.
18 Mutipempherere ife; pakuti takopeka mtima kuti tiri naco cikumbu mtima cokoma m'zonse, pofuna kukhala nao makhalidwe abwino.
19 Ndipo ndikudandaulirani koposa kucita ici, kuti kubwera kwanga kwa inu kufulumidwe.
20 Koma Mulungu wa mtendere amene anabwera naye woturuka mwa akufa 1 Mbusa wamkuru wa nkhosa 2 ndi mwazi wa cipangano cosatha, ndiye Ambuye wathu Yesu,
21 3 akuyeseni inu opanda cirema m'cinthu ciri conse cabwino, kuti mucite cifuniro cacej ndi kucita mwa ife comkondweretsa pamaso pace, mwa Yesu Kristu; kwa Iyeyu ukhale ulemerero ku nthawi za nthawi. Amen.
22 Koma ndidandaulira inu, abale, lolani mau acidandauliro; pakutinso ndalembera inu mwacidule.
23 Zindikirani kuti mbale wathu 4 Timoteo wamasulidwa; pamodzi ndi iye, ngati akudza msanga, ndidzakuonani inu.
24 Lankhulani 5 atsogoleri anu onse, ndi oyera mtima onse. Akulankhulani iwo a ku Italiya.
25 Cisomo cikhale ndi inu nonse. Amen.