1

1 MWEZI wacisanu ndi citatu, caka caciwiri ca Dariyo, mau a Yehova anadza kwa Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido mneneri, ndi kuti,

2 Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.

3 Cifukwa cace uziti nao, Atero Yehova wa makamu: Bwererani kudza kwa Ine, ati Yehova wa makamu, ndipo Ine ndidzabwerera kudza kwa inu, ati Yehova wa makamu.

4 Musamakhala ngati makolo anu, amenie aneneri akale anawapfuulira, nd kuti, Atero Yehova wa makamu Bwereranitu kuleka njira zanu zoipa, ndi macitidwe anu oipa; ko ma sanamva, kapena klimvera Ine ati Yehova.

5 Makolo anu, ali kut iwowo? ndi alieneri, akhala nd moyo kosatha kodi?

6 Koma mau anga ndi malemba anga, amene ndinalamulira atumiki anga aneneriwo, kodi sanawapeza makolo anu? ndipo anabwera, nati, Monga wno Yehova wa makamu analingirira kuticitira ife, monga mwa njira zathu ndi monga mwa macitidwe athu, momwemo anaticitira. Masomphenya oyamba: akavalo,

7 Tsiku la makumi awiri ndi cinai la mwezi wakhumi ndi cimodzi, ndiwo mwezi wa Segati, caka caciwiri ca Dariyo, mau a Yehova anadza kwa Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido mneneri, ndi kuti,

8 Ndinaona usiku, taonani, munthu woyenda pa kavalo wofiira, alikuima pakati pa mitengo yamcisu inali kunsi; ndi pambuyo pace panali akavalo ofiira, odera ndi oyera.

9 Pamenepo ndinati, Awa ndi ciani, mbuyanga? Ndi mthenga wakulankhula ndi ine anati kwa ine, Ndidzakuonetsa awa ndi ciani.

10 Ndipo wakuima pakati pa mitengo yamcisu anayankha, nati, Awa ndiwo amene Yehova anawatumiza ayendeyende m'dziko.

11 Ndipo iwo anamyankha mthenga wa Yehova wakuima pakati pa mitengo yamcisu, nati, Tayendayenda m'dziko, ndipo taonani, dziko lonse likhala cete, lipumula.

12 Ndipo mthenga wa Yehova anayankha nati, Yehova wa makamu, mudzakhala mpaka liti osacitira cifundo Yerusalemu, ndi midzi ya Yuda, imene munakwiya nayo zaka izi makumi asanu ndi awiri?

13 Ndipo Yehova anamyankha mthenga wakulankhula ndi ine mau okoma, mau akutonthoza mtima.

14 Ndipo mthenga wakulankhula ndi ine anati kwa ine, Pfuula, ndi kuti, Atero Yehova wa makamu: Ndicitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni ndi nsanje yaikuru.

15 Ndipo ndikwiya nao amitundu okhala osatekeseka ndi mkwiyo waukuru; pakuti ndinakwiya pang'ono, ndipo anathandizira coipa,

16 Cifukwa cace atero Yehova: Ndabwera kudza ku Yerusalemu ndi zacifundo; nyumba yanga idzamangidwamo, ndipo adzayesa Yerusalemu ndi cingwe.

17 Pfuulanso, ndi kuti, Atero Yehova wa makamu: Midzi yanga idzalemerera ndi kufalikiranso; ndipo Yehova adzasangalatsanso Ziyoni, nadzasankhamo Yerusalemu.

18 Ndipo ndinakweza maso anga, ndinapenya, taonani, nyanga zinai.

19 Ndipo ndinati kwa mthenga wakulankhula ndi ine, Izi nziani? Ndipo anandiyankha, Izi ndi nyangazi zinabalalitsa Yuda, Israyeli, ndi Yerusalemu.

20 Ndipo Yehova anandionetsa osula anai.

21 Pamenepo ndinati, Adzeranji awa? Ndipo ananena, nati, Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, wopandanso wina woweramutsa mutu wace; koma awa anadza kuziopsa, kugwetsa nyanga za amitundu, amene anakwezera dziko la Yuda nyanga zao kulimwaza.

2

1 Ndinakwezanso maso anga, ndinapenya, ndipo taonani, munthu ndi cingwe coyesera m'dzanja lace.

2 Ndipo ndinati, Upita kuti? Ndipo anati kwa ine, Kukayesa Yerusalemu, kuona ngati citando cace ncotani, ndi m'litali mwace motani.

3 Ndipo taonani, mthenga wolankhula nane anaturuka, ndi mthenga wina anaturuka kukomana naye,

4 nanena naye, Thamanga, lankhula ndi mnyamata uyu, ndi kuti, M'Yerusalemu mudzakhala anthu ngati m'midzi yopanda malinga, cifukwa ca kucuruka anthu ndi zoweta momwemo.

5 Pakuti Ine, ati Yehova, ndidzakhala kwa iye linga lamoto pozungulira pace, ndipo ndidzakhala ulemerero m'kati mwace.

6 Haya, haya, thawani ku dziko la kumpoto, ati Yehova; pakuti ndinakubalalitsani ngati mphepo zinai za kuthambo, ati Yehova.

7 Haya Ziyoni, thawa iwe wakukhala ndi mwana wamkazi wa Babulo.

8 Pakuti atero Yehova wa makamu: Utatha ulemererowo ananditumiza kwa amitundu amene anakufunkhani; pakuti iye wokhudza inu, akhudza mwana wa m'diso lace.

9 Pakuti, taonani, ndidzawayambasira dzanja langa, ndipo adzakhala zofunkha za iwo amene anawatumikira; ndipo mudzadziwa kuti Yehova wa makamu anandituma.

10 Yimba, nukondwere, mwana wamkazi wa Ziyoni; pakuti taonani, ndirinkudza, ndipo ndidzakhala pakati pako, ati Yehova.

11 Ndipo amitundu ambiri adzaphatikidwa kwa Yehova tsiku ilo, nadzakhala anthu anga; ndipo ndidzakhala pakati pako, ndipo udzadziwa kuti Yehova wa makamu anandituma kwa iwe.

12 Ndipo Yehova adzalandira colowa cace Yuda, ngati gawo lace m'dziko lopatulikalo, nadzasankhanso Yerusalemu.

13 Khalani cete, anthu onse, pamaso pa Yehova; pakuti wagalamuka mokhalira mwace mopatulika.

3

1 Pamenepo anandionetsa Yoswa mkulu wa ansembe alikuima pamaso pa mthenga wa Yehova, ndi Satana alikuima pa dzanja lace lamanja, atsutsana naye.

2 Ndipo Yehova anati kwa Satana, Yehova akudzudzula, Satana iwe; inde Yehova amene anasankha Yerusalemu akudzudzula; uyu sindiye muuni wofumulidwa kumoto?

3 Koma Yoswa analikubvala nsaru zonyansa, naima pamaso pa mthenga.

4 Ndipo Iye anayankha nanena ndi iwo akuima pamaso pace, ndi kuti, Mumbvule nsaru zonyansazi. Nati kwa iye, Taona, ndakucotsera mphulupulu zako, ndipo ndidzakubveka: zobvala za mtengo wace.

5 Ndipo ndinati, Amuike nduwira yoyera pamutu pace. Naika nduwira yoyera pamutu pace, nambveka ndi zobvala; ndi mthenga wa Yehova anaimirirapo,

6 Ndipo mthenga wa Yehova anamcitira Yoswa umboni, ndi kuti,

7 Atero Yehova wa makamu: Ukadzayenda m'njira zanga, ndi kusunga udikiro wanga, pamenepo udzaweruza nyumba yanga, ndi kusunga mabwalo anga, ndipo ndidzakupatsa malo oyendamo mwa awa oimirirapo.

8 Tamvera tsono, Yoswa mkulu wa ansembe, iwe ndi anzako akukhala pansi pamaso pako; pakuti iwo ndiwo cizindikilo; pakuti taonani, ndidzafikitsa mtumiki wanga, ndiye Mphukira.

9 Pakuti taona, mwalawo ndinauika pamaso pa Yoswa; pa mwala umodzi pali maso asanu ndi awiri; taonani, ndidzaloca malocedwe ace, ati Yehova wa makamu, ndipo ndidzacotsa mphulupulu ya dziko lija tsiku limodzi.

10 Tsiku lomwelo, ati Yehova wa makamu, mudzaitanizana yense mnansi wace patsinde pa mpesa ndi patsinde pa mkuyu.

4

1 Ndipo mthengayo adalankhula nane, anadzanso, nandiutsa ngati munthu woutsidwa m'tulo tace.

2 Ndipo anati kwa ine, Uona ciani? Ndipo ndinati, Ndaona, taonani, coikapo nyali ca golidi yekha yekha, ndi mbale yace pamwamba pace, ndi nyali zace zisanu ndi ziwiri pamenepo; nyalizo zinali ndi misiwe isanu ndi iwiri, ndiyo ya nyalizo zinali pamwamba pace;

3 ndi mitengo iwiri yaazitona pomwepo, wina ku dzanja lamanja la mbaleyo, ndi wina ku dzanja lace lamanzere.

4 Ndipo ndinayankha ndi kunena ndi mthenga wakulankhula ndi ine, ndi kuti, Izi nziani mbuyanga?

5 Ndipo mthenga wakulankhula ndi ine anayankha, nati kwa ine, Sudziwa kodi kuti nziani izi? Ndipo ndinati, Iai, mbuyanga.

6 Pamenepo anayankha, nanena kwa ine, ndi kuti, Awa ndi mau a Yehova kwa Zerubabele, Ndi khamu la nkhondo ai, ndi mphamvu ai, koma ndi Mzimu wanga, ati Yehova wa makamu.

7 Ndiwe yani, phiri lalikuru iwe? pamaso pa Zerubabele udzasanduka cidikha; ndipo adzaturutsa mwala wa cimbudzi, ndi kupfuula, Cisomo, cisomo nao.

8 Ndipo mau a Yehova anadza kwa ine, ndi kuti,

9 Manja a Zerubabele anaika maziko a nyumba iyi, manja ace omwe adzaitsiriza; ndipo udzadziwa kuti Yehova wa makatnu anandituma kwa inu.

10 Pakuti wapeputsa tsiku la tinthu tating'ono ndani? pakuti adzakondwera, asanu ndi awiri awa, nadzaona cingwe colungamitsira ciriri m'dzanja la Zerubabele, ndiwo maso a Yehova; ayendayenda mwa dziko lonse.

11 Pamenepo ndinayankha, ndinati kwa iye, Mitengo iyi iwiri ya azitona kulamanja ndi kulamanzere kwa coikapo nyali nciani?

12 Ndipo ndinayankha kaciwiri, ndinati naye, Nzotani nthambi ziwiri izi za azitona zirikutsanula zokha mafuta onga golidi mwa misiwe iwiri yagolidi?

13 Ndipo anandiyankha, nati, Sudziwa kodi kuti nziani izi? Ndipo ndinati, Iai, mbuyanga.

14 Pamenepo anati, Awa ndi ana amuna awiri a mafuta oimirira pamaso pa Mbuye wa dziko lonse lapansi.

5

1 Pamenepo ndinakwezanso maso anga, ndinapenya, taonani, mpukutu wouluka.

2 Ndipo anati kwa ine, Uona ciani? Ndipo ndinayankha, Ndiona mpukutu wouluka; utali wace mikono makumi awiri, ndi citando cace mikono khumi.

3 Ndipo anati kwa ine, Ili ndi temberero lirikuturukira pa dziko lonse; pakuti ali yense wakuba adzapitikitsidwa kuno monga mwa ili; ndi ali yense wakulumbira zonama adzapitikitsidwa kuno monga mwa ili.

4 Ndidzaliturutsa ili, ati Yehova wa makamu, ndipo lidzalowa m'nyumba ya wakuba, ndi m'nyumba ya iye wolumbira monama pa dzina langa; ndipo lidzakhala pakati pa nyumba yace, ndi kuitha pamodzi ndi mitengo yace ndi miyala yace.

5 Pamenepo mthenga wakulankhula ndi ine anaturuka, nati kwa ine, Kwezatu maso ako, nuone ngati nciani ici cirikuturukaci.

6 Ndipo ndinati, Nciani ici? Nati iye, Ici ndi efa alikuturuka. Natinso, Ici ndi maonekedwe ao m'dziko lonse;

7 (ndipo taonani, cozunguniza cantobvu cotukulidwa) ndipo ici ndi mkazi wokhala pakati pa efa.

8 Ndipo anati, Uyu ndi ucimo; namgwetsa m'kati mwa efa; naponya ntobvu wolemerawo pakamwa pace.

9 Pamenepo ndinakweza maso anga, ndinapenya, ndipo taonani, anaturuka akazi awiri, ndi m'mapiko mwao munali mphepo; ndipo anali nao mapiko ngati mapiko a cumba, nanyamula efayo pakati pa dziko ndi thambo.

10 Ndipo ndinati kwa mthenga wakulankhula ndi ine, Amenewa amuka naye kuti efayo?

11 Ndipo anati kwa ine, Kummangira nyumba m'dziko la Sinara; kuti amuike, namkhazikeko pa kuzika kwace.

6

1 Ndipo ndinakwezanso maso anga, ndinapenya, ndipo taonani, anaturuka magareta anai pakati pa mapiri awiri; ndi mapiriwo ndiwo mapiri amkuwa.

2 Ku gareta woyamba kunali akavalo ofiira; ndi ku gareta waciwiri akavalo akuda;

3 ndi ku gareta wacitatu akavalo oyera; ndi ku gareta wacinai akavalo olimba amawanga.

4 Ndipo ndinayankha ndinati kwa mthenga wolankhula ndi ine, Izi nziani, mbuyanga?

5 Ndi mthenga anayankha, nati kwa ine, Izi ndi mphepo zinai zakumwamba zakuturuka kumene zimaimirira pamaso pa Ambuye wa dziko lonse lapansi.

6 Gareta wa akavalo akuda aturukira ku dziko la kumpoto; ndi oyerawo aturukira kuwatsata; ndi amawanga aturukira ku dziko la kumwela.

7 Ndi amphamvuwo anaturuka nayesa kumka kuyendayenda m'dziko; pakuti adati, Mukani, yendayendani m'dziko. Momwemo anayendayenda m'dziko.

8 Ndipo anandiitana, nanena nane, kuti, Taonani, iwo akuturuka kumka ku dziko la kumpoto anapumulitsa Mzimu wanga m'dziko lakumpoto.

9 Ndipo mau a Yehova anadza kwa ine, ndi kuti,

10 Tenga a iwo a kundende, a Keledai, a Tobiya, ndi a Yedaya; nudze tsiku lomwelo, nulowe ku nyumba ya Yosiya, mwana wa Zefaniya, kumene anafikirako kucokera ku Babulo,

11 ndipo utenge siliva ndi golidi, nupange akorona, nuwaike pamutu pa Yoswa mwana wa Yehozadaki mkuru wa ansembe;

12 nunene naye, kuti, Atero Yehova wa makamu, ndi kuti, Taonani, munthu dzina lace ndilo Mphukira, ndipo adzaphuka m'malo mwace, nadzamanga Kacisi wa Yehova:

13 inde adzamanga Kacisi wa Yehova; nadzasenza ulemererowo, nadzakhala ndi kulamulira pa mpando wacifumu wace; nadzakhala wansembe pampando wacifumu wace; ndi uphungu wa mtendere udzakhala pakati pa iwo awiri,

14 Ndipo akorona adzakhala wa Kelemu, ndi wa Tobiya, ndi wa Yedaya, ndi wa Keni mwana wa Zefaniya, akhale cikumbutso m'Kacisi wa Yehova.

15 Ndipo iwo akukhala kutari adzafika, nadzamanga ku Kacisi wa Yehova, ndipo inu mudzadziwa kuti Yehova wa makamu ananditumiza kwa inu. Ndipo ici cidzacitika ngati mudzamvera mwacangu mau a Yehova Mulungu wanu.

7

1 Ndipo kunacitika caka cacinai ca mfumu Dariyo, mau a Yehova anadza kwa Zekariya tsiku lacinai la mwezi wacisanu ndi cinai, ndiwo Kisilevi.

2 Ndipo a ku Beteli anatuma Sarezere ndi Regemeleke ndi anthu ao, apepeze Yehova,

3 nanene kwa ansembe a nyumba ya Yehova wa makamu, ndi kwa aneneri, ndi kuti, Kodi ndilire mwezi wacisanu, ndi kudzipatula, monga umo ndikacitira zaka izi zambiri?

4 Ndipo mau a Yehova wa makamu anadza kwa ine, ndi kuti,

5 Nena kwa anthu onse a m'dziko, ndi kwa ansembe, kuti, Muja mukasala ndi kulira mwezi wacisanu, ndi wacisanu ndi citatu, zaka izi makumi asanu ndi awiri, kodi mukasalira Ine, Inedi?

6 Ndipo pamene mukadya, ndi pamene mukamwa, mukadya si ndinu, mukamwa si ndinu kodi?

7 Si ndiwo mau Yehova anawalalikira mwa aneneri oyamba aja, muja Yerusalemu anali nao okhalamo, ndi wokhazikika; ndi m'midzi mwace pozungulira pace, ndi m'dziko la kumwela, ndi m'cidikha munali anthu okhalamo?

8 Ndipo mau a Yehova anadza kwa Zekariya, ndi kuti,

9 Watero Yehova wa makamu, kuti, Weruzani ciweruzo coona, nimucitire yense mnzace cifundo ndi ukoma mtima;

10 musazunza mkazi wamasiye, kapena ana amasiye, mlendo kapena waumphawi; ndipo nnena mmodzi wa inu alingirire m'mtima mwace kumcitira coipa munthu mnzace.

11 Koma anakana kumvera, nakaniza phewa lao, natseka makutu ao, kuti asamve.

12 Inde, anasanduliza mitima yao ikhale ngati mwala woti gwa, kuti angamve cilamulo, ndi mau amene Yehova wa makamu anatumiza ndi Mzimu wace mwa aneneri oyamba aja; m'menemo munafuma mkwiyo waukuru wocokera kwa Yehova wa makamu.

13 Ndipo kunacitika, monga Iye anapfuula, koma iwo sanamvera; momwemo iwo adzapfuula, koma Ine sindidzamva, ati Yehova wa makamu;

14 koma ndidzawabalalitsa ndi kabvumvulu mwa amitundu onse amene sanawadziwa. Motero dziko linakhala bwinja, m'mbuyo mwao; palibe munthu wopitapo ndi kubwererako; pakuti adaika dziko lofunikalo labwinja.

8

1 Ndipo mau a Yehova wa makamui anadza kwa ine, ndi kuti,

2 Atero Yehova wa makamu: Ndimcitira nsanje Ziyoni ndi nsanje yaikuru, ndipo ndimcitira nsanje ndi ukali waukuru.

3 Atero Yehova: Ndabwerera kudza ku Ziyoni, ndidzakhala pakati pa Yerusalemu; ndi Yerusalemu adzachedwa, Madzi wa coonadi; ndi phiri la Yehova wa makamu, Phiri lopatulika.

4 Atero Yehova wa makamu: M'miseu ya Yerusalemu mudzakhalanso amuna ndi akazi okalamba, yense ndi ndodo yace m'dzanja lace cifukwa ca ukalamba wace.

5 Ndi m'miseu ya mudzi mudzakhala ana amuna ndi akazi akusewera m'miseu yace.

6 Atero Yehova wa makamu: Cikakhala codabwitsa pamaso pa otsala a anthu awa masiku awo, kodi cidzakhalanso codabwitsa pamaso panga? ati Yehova wa makamu.

7 Atero Yehova wa makamu: Taonani, ndidzapulumutsa anthu anga m'dziko la kum'mawa, ndi m'dziko la kumadzulo;

8 ndipo ndidzabwera nao, nadzakhala m'kati mwa Yerusalemu; ndipo iwo adzakhala anthu anga, nanenso ndidzakhala Mulungu wao, m'coonadi ndi m'cilungamo.

9 Atero Yehova wa makamu: Alimbike manja anu, inu akumva masiku ano mau awa pakamwa pa aneneri amene anakhalako tsiku lakuikidwa maziko a nyumba ya Yehova wa makamu, ndiyo Kacisi, kuti amangidwe.

10 Pakuti asanafike masiku aja, panalibe kulipidwira munthu, kapena kulipidwira nyama, ndipo analibe mtendere iye wakuturuka, kapena wakulowa, cifukwa ca wosautsa; pakuti ndinatumiza munthu yense atsutsane naye mnzace.

11 Koma tsopano sindidzakhala kwa otsala a anthu awa monga momwe ndinakhalira masiku oyamba, ati Yehova wa makamu.

12 Pakuti padzakhala mbeu ya mtendere; mpesa udzapatsa zipatso zace, ndi nthaka idzapatsa zobala zace, ndi miyamba Idzapatsa mame ao; ndipo ndidzalandiritsa otsala a anthu awa izi zonse, cikhale colowa cao.

13 Ndipo kudzacitika kuti, monga munali cotembereretsa mwa amitundu, inu nyumba ya Yuda, ndi nyumba ya Israyeli, momwemo ndidzakusungani, ndipo mudzakhala codalitsa naco; musaope, alimbike manja anu.

14 Pakuti atero Yehova wa makamu: Monga ndil nalingirira kucitira inu coipa, muja makolo anu anautsa mkwiyo wanga, ati Yehova wa makamu, ndipo sindinawaleka;

15 momwemonso ndinalingirira masiku ano kucitira cokoma Yerusalemu ndi nyumba ya Yuda; musaopa.

16 Izi ndizo muzicite: Nenani coonadi yense ndi mnzace; weruzani zoona ndi ciweruzo ca mtendere m'zipata zanu;

17 ndipo musalingirira coipa m'mtima mwanu yense pa mnzace; nimusakonde lumbiro lonama; pakuti izi zonse ndidana nazo, ati Yehova.

18 Ndipo mau a Yehova wa makamu anadza kwa ine, ndi kuti,

19 Atero Yehova wa makamu: Kusala kwa mwezi wacinai, ndi kusala kwa mwezi wacisanu, ndi kusala kwa mwezi wacisanu ndi ciwiri, ndi kusala kwa mwezi wakhumi kukhale kwa nyumba ya Yuda cimwemwe ndi cikondwerero, ndi nyengo zoikika zosekerera; cifukwa cace kondani coonadi ndi mtendere.

20 Atero Yehova wa makamu: Kudzacitikanso kuti mitundu ya anthu, ndi okhalamo m'midzi yambiri adzafika,

21 ndi okhala m'mudzi umodzi adzamuka ku mudzi wina, ndi kuti, Tiyeni msanga kukapepeza Yehova, ndi kufunafuna Yehova wa makamu; ndimuka inenso.

22 Inde, mitundu yambiri ya anthu, ndi amitundu amphamvu adzadza kufunafuna Yehova wa makamu m'Yerusalemu, ndi kupepeza Yehova.

23 Atero Yehova wa makamu: Kudzacitika masiku awo amuna khumi adzagwira, ndiwo a manenedwe onse a amitundu, inde adzagwira mkawo wa munthu ali Myuda, ndi kuti, Tidzamuka nanu, pakuti tamva kuti Mulungu ali ndi inu.

9

1 Katundu wa mau a Yehova pa dziko la Hadraki, ndipo Damasiko adzakhala popumula pace; pakuti Yehova apenyerera anthu monga apenyerera mafuko onse a Israyeli;

2 ndi Hamati yemwe wogundana naye malire; Turo ndi Zidoni, angakhale ali ndi nzeru zambiri.

3 Ndipo Turo adzadzimangira polimbikirapo, nadzakundika siliva ngati pfumbi, ndi golidi woyenga ngati thope la kubwalo.

4 Taonani, Yehova adzamlanda zace, nadzakantha mphamvu yace igwe m'manja; ndipo adzatha ndi moto.

5 Asikeloni adzaciona, nadzaopa; Gazanso, nadzanjenjemera kwambiri; ndi Ekroni, pakuti ciyembekezo cace cacitidwa manyazi; ndipo mfumu idzatayika ku Gaza, ndi Asikeloni adzasowa okhalamo.

6 Ndi mtundu wa anthu osokonezeka udzakhala m'Asidodi, ndipo ndidzaononga kudzikuza kwa Afilisti.

7 Ndipo ndidzacotsa mwazi wace m'kamwa mwace, ndi zonyansa zace pakati pa mano ace; momwemo iyenso adzakhala wotsalira wa Mulungu wathu, ndipo adzakhala ngati mkuru wa pfuko m'Yuda, ndi Ekroni ngati Myebusi.

8 Ndipo ndidzamangira nyumba yanga misasa, kuiletsera nkhondo, asapitepo munthu kapena kubweranso; ndipo wakuwasautsa sadzapitanso pakati pao; pakuti tsopano ndapenya ndi maso anga.

9 Kondwera kwambiri, mwana wamkazi wa Ziyoni; pfuula mwana wamkazi wa Yerusalemu; taona, Mfumu yako ikudza kwa iwe; ndiye wolungama, ndi mwini cipulumutso; wofatsa ndi wokwera pa buru, ndi mwana wamphongo wa buru.

10 Ndipo ndidzaononga magareta kuwacotsa m'Efraimu, ndi akavalo kuwacotsa m'Yerusalemu; ndi uta wa nkhondo udzaonongeka; ndipo adzanena zamtendere kwa amitundu; ndi ufumu wace udzakhala kuyambira kunyanja kufikira nyanja, ndi kuyambira ku Mtsinje kufikira malekezero a dziko.

11 Iwenso, cifukwa ca mwazi wa pangano lako ndinaturutsa andende ako m'dzenje m'mene mulibe madzi.

12 Bwererani kudza kulinga, andende a ciyembekezo inu; ngakhale lero lino ndilalikira kuti ndidzakubwezera cowirikiza.

13 Pakuti ndadzikokera Yuda, ndadzaza uta ndi Efraimu; ndipo ndidzautsa ana ako, Ziyoni, alimbane nao ana ako, Yavani, ndipo ndidzakuyesa lupanga la ngwazi.

14 Ndipo Yehova adzaoneka pamwamba pao, ndi mubvi wace udzaturuka ngati mphezi; ndipo Ambuye Mulungu adzaomba lipenga, nadzayenda ndi akabvumvulu a kumwela.

15 Yehova wa makamu adzawacinjiriza; ndipo adzadza, nadzapondereza miyala yoponyera; ndipo adzamva, nadzacita phokoso ngati avinyo; ndipo adzadzazidwa ngati mbale, ngati ngondya za guwa la nsembe.

16 Ndipo Yehova Mulungu wao adzawapulumutsa tsiku ilo, ngati zoweta za anthu ace; pakuti adzakhala ngati miyala ya m'korona yakunyezimira pa dziko lace.

17 Pakuti ukoma wace ndi waukuru ndithu, ndi kukongola kwace nkwa kukuru ndithu! tirigu adzakometsera anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.

10

1 Pemphani kwa Yehova mvula, m'nyengo ya mvula ya masika, kwa Yehova wolenga mphezi; ndipo adzawapatsa mibvumbi ya mvula, kwayense zophukira kuthengo.

2 Pakuti aterafi anena zopanda pace, ndi aula aona bodza; nafotokoza maloto acabe, asangalatsa nazo zopanda pace; cifukwa cace ayendayenda ngati nkhosa, azunzika popeza palibe mbusa.

3 Mkwiyo wanga wayakira abusa, ndipo ndidzalanga atonde; pakuti Yehova wa makamu adzazonda zoweta zace, ndizo nyumba ya Yuda, nadzaziika ngati kavalo wace waulemerero kunkhondo.

4 Kwa iye kudzafuma mwala wa kungondya, kwa iye msomali, kwa iye uta wankhondo, kwa iye osautsa onse pamodzi.

5 Ndipo adzakhala ngati ngwazi zakupondereza adani m'thope la kubwalo kunkhondo; ndipo adzacita nkhondo, cifukwa Yehova ali nao; ndi apakavalo adzacitidwa manyazi.

6 Ndipo ndidzalimbitsa nyumba ya Yuda, ndi kusunga nyumba ya Yosefe, ndipo ndidzawakhalitsa, pakuti ndawacitira cifundo; ndipo adzakhala monga ngati sindinawataya konse; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wao, ndipo ndidzawamvera.

7 Ndipo iwo a ku Efraimu adzakhala ngati ngwazi, ndi mtima wao udzakondwera ngati ndi vinyo; ndipo ana ao adzaciona nadzakondwera; mtima wao udzakondwerera mwa Yehova.

8 Ndidzawayimbira mluzu ndi kuwasonkhanitsa, pakuti ndawaombola; ndipo adzacuruka monga anacurukira kale.

9 Ndipo ndidzawafesa mwa mitundu ya anthu, ndipo adzandikumbukila m'maiko akutali; nadzakhala pamodzi ndi ana ao, nadzabwera.

10 Ndidzawatenganso ku dziko la Aigupto, ndi kuwasonkhanitsa m'Asuri; ndipo ndidzalowa nao m'dziko la Gileadi ndi Lebano; koma sadzawafikira.

11 Ndipo adzapita pakati pa nyanja ya nsautso, nadzapanda mafunde a m'nyanja, ndi maiwe onse a mtsinje adzaphwa; ndi kudzikuza kwa Asuri kudzagwetsedwa; ndi ndodo yacifumu ya Aigupto idzacoka.

12 Ndipo ndidzawalimbitsa mwa Yehova; ndipo adzayendayendam'dzina lace, ati Yehova.

11

1 Tsegula pa makomo ako Lebano, kuti moto uthe mikungudza yako.

2 Cema, mtengo wamlombwa, pakuti mkungudza wagwa, popeza mitengo yokoma yaipitsidwa; cemani athundu a ku Basani, pakuti nkhalango yocinjirizika yagwa pansi.

3 Mau a kucema kwa abusa! pakuti ulemerero wao waipsidwa; mau a kubangula kwa misona ya mikango! pakuti kudzikuza kwa Yordano kwaipsidwa.

4 Atero Yehova Mulungu wanga: Dyetsani zoweta zakukaphedwa;

5 zimene eni ace azipha, nadziyesera osaparamula; ndi iwo akuwagulitsa akuti, Alemekezedwe Yehova, pakuti ine ndine wolemera; ndi abusa ao sazicitira cifundo.

6 Pakuti sindidzacitiranso cifundo okhala m'dzikomo, ati Yehova; koma taonani, ndidzapereka anthu, yense m'dzanja la mnansi wace, ndi m'dzanja la mfumu yace; ndipo iwo adzakantha dzikoli, ndi m'dzanja mwao sindidzawalanditsa.

7 M'mwemo ndinadyetsa zoweta zakukaphedwa, ndizo zoweta zonyankhalala. Ndipo ndinadzitengera ndodo ziwiri; yina ndinaicha Cisomo, inzace ndinaicha Comanganitsa; ndipo ndinadyetsa zowetazo.

8 Ndipo ndinatha abusa atatuwo mwezi umodzi; pakuti mtima wanga unalema nao, ndi mtima waonso unaipidwa nane.

9 Pamenepo ndinati, Sindidzadyetsanso inu; cirikufa cife; cosoweka cisoweke; ndi zotsala zidyane, conse nyama ya cinzace.

10 Ndipo ndinatenga ndodo yanga Cisomo, ndi kuidula pakati, kuti ndiphwanye pangano langa ndinalicita ndi mitundu yonse ya anthu.

11 Ndipo linatyoka tsikulo, momwemo zonyankhalala za zoweta, zakundisamalira Ine, zinadziwa kuti ndiwo mau a Yehova.

12 Ndipo ndinanena nao, Cikakomera inu, ndipatseni mphotho yanga; ngati iai, lekani. Ndipo anayesa mphotho yanga, kulemera kwace ndarama zasiliva makumi atatu.

13 Ndipo Yehova anati kwa ine, Kaziponye kwa woumba mbiya, mtengo wace wokometsetsa anandiyesawo. Ndipo ndinatenga ndarama makumi atatu asiliva, ndi kuziponya kwa woumba mbiya, m'nyumba ya Yehova.

14 Pamenepo ndinadula ndodo yanga yina, ndiyo Comanganitsa, kuti ndithetse cibale ca pakati pa Yuda ndi Israyeli.

15 Ndipo Yehova anati kwa ine, Dzitengerenso zipangizo za mbusa wopusa.

16 Pakuti taonani, ndidzautsa mbusa m'dziko amene sadzazonda otayika, kapena kufunafuna zomwazika, kapena kulunzitsa yotyoka, kapena kudyetsa yamoyo, koma adzadya nyama ya zonenepa, nadzang'amba ziboda zao.

17 Tsoka mbusa wopanda pace, wakusiya zoweta! lupanga pa dzanja lace, ndi pa diso lace la kumanja; dzanja lace lidzauma konse, ndi diso lace lamanja lidzada bii.

12

1 Katundu wa mau a Yehova wakunena Israyeli. Atero Yehova, wakuyala miyamba, ndi kuika maziko a dziko lapansi, ndi kulenga mzimu wa munthu m'kati mwace;

2 Taonani, ndidzaika Yerusalemu akhale cipanda codzandiritsa kwa mitundu yonse ya anthu yozungulirapo, ndipo cidzafikira Yuda yemwe pomangira misasa Yerusalemu.

3 Ndipo kudzacitika tsiku ilo, ndidzaika Yerusalemu akhale mwala wolemetsa mitundu yonse ya anthu; onse akuusenza adzadzilasa nao; ndi amitundu onse a pa dziko lapansi adzasonkhana kutsutsana nao.

4 Tsiku ilo, ati Yehova, ndidzakantha kavalo ali yense ndi kumdabwitsa, ndi womkwera adzayaluka; ndipo ndidzatsegulira maso anga nyumba ya Yuda, ndi kukantha kavalo ali yense wa mitundu ya anthu akhale wakhungu.

5 Ndipo akalonga a Yuda adzanena m'mtima mwao, Okhala m'Yerusalemu ndiwo mphamvu yanga m'Yehova wa makamu Mulungu wao.

6 Tsiku ilo ndidzaika akalonga a Yuda ngati phale la moto pansi pa nkhuni, ndi ngati muuni wamoto mwa mitolo ya tirigu; ndipo adzatha mitundu yonse ya anthu pozungulirapo, ku dzanja lamanja ndi lamanzere; ndipo Yerusalemu adzakhalanso m'malo mwace, m'Yerusalemu.

7 Ndipo Yehova adzayamba kupulumutsa mahema a Yuda, kuti ulemerero wa nyumba ya Davide ndi ulemerero wa okhala m'Yerusalemu usakulire Yuda.

8 Tsiku ilo Yehova adzacinjiriza okhala m'Yerusalemu; ndi iye wokhumudwa pakati pao tsiku lomwelo adzakhala ngati Davide; ndi nyumba ya Davide idzakhala ngati Mulungu, ngati mthenga wa Yehova pakati pao.

9 Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo, ndidzayesa kuononga amitundu onse akudza kuyambana ndi Yerusalemu.

10 Ndipo ndidzatsanulira pa nyumba ya Davide, ndi pa okhala m'Yerusalemu, mzimu wa cisomo ndi wakupembedza; ndipo adzandipenyera Ine amene anandipyoza; nadzamlira ngati munthu alira mwana wace mmodzi yekha, nadzammvera zowawa mtima, monga munthu amvera zowawa mtima mwana wace woyamba.

11 Tsiku lomwelo kudzakhala maliro akuru m'Yerusalemu, ngati maliro a Hadadirimoni m'cigwa ca Megidoni,

12 Ndipo dziko lidzalira, banja liri lonse pa lokha; banja la nyumba ya Davide pa lokha, ndi akazi ao pa okha; banja la nyumba ya Natani pa lokha, ndi akazi ao pa okha;

13 banja la nyumba ya Levi pa lokha, ndi akazi ao pa lokha; banja la Asimei pa okha, ndi akazi ao pa okha;

14 mabanja onse otsala, banja liri lonse pa lokha, ndi akazi ao pa okha.

13

1 Tsiku lomwelo padzatsegukira nyumba ya Davide ndi okhala m'Yerusalemu kasupe wa kwa ucimo ndi cidetso.

2 Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo, ati Yehova wa makamu, ndidzaononga maina a mafano m'dziko; ndipo sadzakumbukikanso; ndipo ndidzacotsa m'dziko aneneri ndi mzimu wacidetso.

3 Ndipo kudzacitika, akaneneranso wina, atate wace ndi mai wace ombala adzanena naye, Sudzakhala ndi moyo, pakuti unena bodza m'dzina la Yehova; ndipo atate wace ndi mai wace ombala adzamgwaza ponenera iye.

4 Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo kuti aneneri adzacita manyazi yense ndi masomphenya ace, ponenera iye; ndipo sadzabvala copfunda caubweya kunyenga naco;

5 koma adzati, Sindiri mneneri, ndiri wolima munda; pakuti munthu anandiyesa kapolo kuyambira ubwana wanga.

6 Ndipo wina akati kwa iye, Zipsera izi m'manja mwako nza ciani? adzayankha, Ndizo za mabala anandilasa m'nyumba ya ondikonda.

7 Galamuka, lupanga, pa mbusa wanga, ndi pa munthu mnzanga wa pamtima, ati Yehova wa makamu; kantha mbusa, ndi nkhosa zidzabalalika; koma ndidzabwezera dzanja langa pa zazing'onozo.

8 Ndipo kudzacitika m'dziko lonse, ati Yehova, magawo awiri m'menemo adzalikhidwa nadzafa; koma gawo lacitatu lidzasiyidwa m'mwemo.

9 Ndi gawo lacitatulo ndidzalitengera kumoto, ndi kuwayenga ngati ayenga siliva, ndi kuwayesa monga ayesa golidi; adzaitana dzina langa, ndipo ndidzawamvera; ndidzati, Awa ndi anthu anga; ndi iwo adzati, Yehova ndi Mulungu wanga.

14

1 Taonani likudza tsiku la Yehova, limene zofunkha zako zidzagawanika pakati pako.

2 Pakuti ndidzasonkhanitsa amitundu onse alimbane ndi Yerusalemu; ndipo mudziwo udzalandidwa, ndi nyumba zidzafunkhidwa, ndi akazi adzakakamizidwa; ndi limodzi la magawo awiri la mudzi lidzaturuka kumka kundende, koma anthu otsala sadzaonongeka m'mudzimo.

3 Pamenepo Yehova adzaturuka, nadzacita nkhondo ndi amitundu aja, monga anacitira nkhondo tsiku lakudumana.

4 Ndi mapazi ace adzaponda tsiku lomwelo pa phiri la Azitona, liri pandunji pa Yerusalemu kum'mawa, ndi phiri la Azitona lidzang'ambika pakati kuloza kum'mawa ndi kumadzulo, ndipo padzakhala cigwa cacikuru; ndi gawo lina la phirilo lidzamuka kumpoto, ndi gawo lina kumwela.

5 Pamenepo mudzathawa kudzera cigwa ca mapiri anga; pakuti cigwa ca mapiri cidzafikira ku Azali; ndipo mudzathawa monga umo munathawira cibvomezi, masiku a Uziya mfumu ya Yuda; ndipo Yehova Mulungu wanga adzadza, ndi opatulika onse pamodzi ndi Inu.

6 Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo, sikudzakhala kuunika, zowalazo zidzada;

7 koma lidzakhala tsiku la pa lokha lodziwika ndi Yehova; palibe usana, palibe usiku; koma kudzatero kuti madzulo kudzati mbe.

8 Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo kuti madzi amoyo adzaturuka ku Yerusalemu; gawo lao lina kumka ku nyanja ya kum'mawa, ndi gawo lina kumka ku nyanja ya kumadzulo; adzatero nyengo ya dzinja ndi ya mwamvu.

9 Ndipo Yehova adzakhala mfumu ya dziko lonse; tsiku lomwelo Yehova adzakhala Iye yekha, ndi dzina lace ilo lokha.

10 Dziko lonse lidzasandulika, lidzanga cidikha, kuyambira ku Geba kufikira ku Rimoni, kumwela kwa Yerusalemu; ndipo pali uwupo padzakhala ponyamuka, ndipo udzakhala m'malo mwace, kuyambira ku cipata ca Benjamini kufikira ku malo a cipata coyamba, kufikira ku cipata ca kungondya, ndi kuyambira nsanja ya Hananeli kufikira ku zoponderamo mphesa za mfumu.

11 Ndipo anthu adzakhala m'menemo, ndipo sipadzakhalanso kuonongetsa; koma Yerusalemu adzakhala mosatekeseka.

12 Ndipo mliri umene Yehova adzakantha nao mitundu yonse ya anthu imene idathira nkhondo pa Yerusalemu ndi uwu: nyama yao idzaonda akali ciriri pa mapazi ao, ndi maso ao adzapuala m'pfunkha mwao, ndi lilime lao lidzanyala m'kamwa mwao.

13 Ndipo kudzali tsiku lomwelo, kuti cisokonezo cacikuru cocokera kwa Yehova cidzakhala pakati pao; ndipo adzagwira yense dzanja la mnzace; ndi dzanja lace lidzaukira dzanja la mnzace.

14 Ndi Yuda yemwe adzacita nkhondo ku Yerusalemu; ndi zolemera za amitundu onse ozungulirapo zidzasonkhanizidwa, golidi, ndi siliva, ndi zobvala zambirimbiri.

15 Momwemonso mliri wa pa akavalo, nyuru, ngamila, ndi aburu, ndi nyama zonse zokhala m'misasa iyo, udzakhala ngati mliri uwo.

16 Ndipo kudzacitika kuti otsala onse a amitundu onse anadzawo kulimbana ndi Yerusalemu, adzakwera caka ndi caka kulambira mfumu Yehova wa makamu, ndi kusunga madyerero amisasa.

17 Ndipo kudzacitika kuti ali yense wa mabanja a dziko wosakwera kumka ku Yerusalemu kulambira mfumu Yehova wa makamu, pa iwowa sipadzakhala mvula.

18 Ndipo banja la ku Aigupto likapanda kukwera, losafika, sirdzawagwera kodi mliri umene Yehova adzakantha nao amitundu osakwera kusunga madyerero amisasa?

19 Ili ndi cimo la Aigupto, ndi cimo la amitundu onse osakwerako kusunga madyerero a misasa.

20 Tsiku lomwelo padzaoneka pa miriu ya akavalo OPATULIKIRA YEHOVA; ndi mbiya za m'nyumba ya Yehova zidzanga mbale za ku guwa la nsembe.

21 Inde mbiya zonse za m'Yerusalemu ndi m'Yuda zidzakhala zopatulikira Yehova wa makamu; ndi onse akuphera nsembe adzafika nadzatengako, ndi kuphikamo; ndipo tsiku lomwelo simudzakhalanso Mkanani m'nyumba ya Yehova wa makamu.