1 MAU a Yehova a kwa Yoeli mwana wa Petueli.
2 Imvani ici, akulu akulu inu, nimuchere khutu, inu nonse okhala m'dziko. Cacitika ici masiku anu kodi, kapena masiku a makolo anu?
3 Mufotokozere ana anu ici, ndi ana anu afotokozere ana ao, ndi ana ao afotokozere mbadwo wina.
4 Cosiya cimbalanga, dzombe lidacidya; ndi cosiya dzombe, cirimamine adacidya; ndi cosiya cirimamine, anoni adacidya.
5 Galamukani, oledzera inu, nimulire; bumani, nonse akumwa vinyo, cifukwa ca vinyo watsopano; pakuti waletsedwa pakamwa panu.
6 Pakuti mtundu wadza, wakwerera dziko langa, wamphamvu wosawerengeka, mano ace akunga mano a mkango, nukhala nao mano acibwano a mkango waukuru.
7 Unaonongadi mpesa wanga, nunyenya mkuyu wanga, nuukungudza konse, nuutaya; nthambi zace zasanduka zotumbuluka.
8 Lirani ngati namwali wodzimangira m'cuuno ciguduli, cifukwa ca mwamuna wa unamwali wace.
9 Nsembe yaufa ndi nsembe yothira zalekeka ku nyumba ya Yehova; ansembe, atumiki a Yehova, acita maliro.
10 M'munda mwaonongeka, nthaka ilira; pakuti tirigu waonongeka, vinyo watsopano wamwelera, mafuta akudza pang'onong'ono.
11 Gomani, akulima m'minda inu; lirani, akulima mpesa; cifukwa ca tirigu ndi barele; pakuti dzinthu za m'minda zatayika.
12 Mpesa wauma, mkuyu wafota, mtengo wa mkangaza ndi kanjedza ndi muula, inde mitengo yonse ya kuthengo yafota; pakuti cimwemwe cathera ana a anthu.
13 Mudzimangire ciguduli m'cuuno mwanu, nimulire ansembe inu; bwnani, otumikira ku guwa la nsembe inu; lowani, gonani usiku wonse m'ciguduli, inu otumikira Mulungu wanga; pakuti nsembe yaufa ndi nsembe yothira zaletsedwera nyumba ya Mulungu wanu.
14 Patulani tsiku losala, lalikirani masonkhano oletsa, sonkhanitsani akulu akulu, ndi onse okhala m'dziko, ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu; nimupfuulire kwa Yehova.
15 Kalanga ine, tsikuli! pakuti layandikira tsiku la Yehova, lidzafika ngati cionongeko cocokera kwa Wamphamvuyonse.
16 Cakudya sicicotsedwa kodi pamaso pathu? cimwemwe ndi cikondwerero pa nyumba ya Mulungu wathu?
17 Mbeu zaola pansi pa zibuluma zao; zosungiramo zaonongeka, nkhokwe zapasuka; pakuti tirigu wakwinyata.
18 Ha! nyama ziusa moyo, magulu a ng'ombe azimidwa; pakuti zisowa podyera; magulu a nkhosa omwe atha.
19 Ndipfuulira kwa Inu Yehova, pakuti moto wapsereza mabusa a m'cipululu, ndi malawi a moto anatentha mitengo yonse ya kuthengo,
20 inde nyama za kuthengo zilira kwa Inu; pakuti mitsinje yamadzi yaphwa, ndi moto wapsereza mabusa a m'cipululu.
1 Muombe lipenga m'Ziyoni, nimupfuulitse m'phiri langa lopatulika; onse okhala m'dziko anjenjemere; pakuti tsiku la Yehova lirinkudza, pakuti liyandikira;
2 tsiku la mdima, la mdima wandiweyani, tsiku la mitambo, mitambo yocindikira, ngati m'mbandakuca moyalika pamapiri; mtundu waukuru ndi wamphamvu, panalibe wotere ndi kale lonse, sipadzakhalanso wotere utapita uwu, kufikira zaka za mibadwo yambiri.
3 Moto unyambita pamaso pao, ndi m'mbuyo mwao litentha lawi la moto; kumaso kwao dziko likunga munda wa Edeni, koma m'mbuyo mwao likunga cipululu copanda kanthu; palibenso wakuwapulumuka.
4 Maonekedwe ao aoneka ngati akavalo, nathamanga ngati akavalo a nkhondo.
5 Atumphako ngati mkokomo wa magareta pamwamba pa mapiri, ngati kulilima kwa malawi a moto akupsereza ziputu, ngati mtundu wamphamvu wa anthu ondandalikira nkhondo.
6 Pamaso pao mitundu ya anthu ikumva zowawa, nkhope zonse zitumbuluka.
7 Athamanga ngati amphamvu; akwera linga ngati anthu a nkhondo; niliyenda liri lonse njira yace, osasokonezeka m'mabande ao.
8 Sakankhana, ayenda liri lonse m'mopita mwace; akagwa m'zida, siityoka nkhondo yao.
9 Alumphira mudzi, athamanga palinga, akwerera nyumba, alowera pamazenera ngati mkhungu.
10 Dziko lapansi linjenjemera pamaso pao, thambo ligwedezeka, dzuwa ndi mwezi zada, ndi nyenyezi zi'bweza kuwala kwao;
11 ndipo Yehova amveketsa mau ace pamaso pa khamu lace la nkhondo; pakuti a m'cigono mwace ndi ambirimbiri; pakuti Iye wakucita mau ace ndiye wamphamvu ndithu; pakuti tsiku la Yehova ndi lalikuru ndi loopsa ndithu; akhoza kupirira nalo ndani?
12 Koma ngakhale tsopano, ati Yehova, munditembenukire Ine ndi mtima wanu wonse, ndi kusala, ndi kulira, ndi kucita maliro;
13 ndipo ng'ambani mitima yanu, si zobvala zanu ai; ndi kurembenukira kwa Yehova Mulungu wanu; pakuti Iye ndiye wacisomo, ndi wodzala cifundo, wosapsa mtima msanga, ndi wocuruka kukoma mtima, ndi woleka coipaco.
14 Kaya, kapena adzabwerera, nadzalekerera, ndi kusiya mdalitso pambuyo pace, ndiwo nsembe yaufa ndi nsembe yathira ya Yehova Mulungu wanu.
15 Ombani lipenga m'Ziyoni, patulani tsiku losala, lalikirani msonkhano woletsa,
16 sonkhanitsani anthu, patulani msonkhano, memezani akulu akulu, sonkhanitsani ana ndi oyamwa mawere; mkwati aturuke m'cipinda mwace, ndi mkwatibwi m'mogona mwace.
17 Ansembe, atumiki a Yehova, alire pakati pa khonde la pakhomo ndi guwa la nsembe, nanene, Alekeni anthu anu, Yehova, musapereka colowa canu acitonze, kuti amitundu awalamulire; adzaneneranji mwa anthu, Ali kuti Mulunguwao?
18 Pamenepo Yehova anacitira dziko lace nsanje, nacitira anthu ace cifundo.
19 Ndipo Yehova anayankha, nati kwa anthu ace, Taonani, ndidzakutumizirani tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta; ndipo mudzakhuta ndi izo; ndipo sindidzakuperekaninso mukhale citonzo mwa amitundu;
20 koma ndidzakucotserani kutali nkhondo ya kumpoto, ndi kulingira ku dziko louma ndi lopasuka, a kumaso kwace ku nyanja ya kum'mawa, ndi a kumbuyo kwace ku nyanja ya kumadzulo; ndi kununkha kwace kudzakwera, ndi pfungo lace loipa lidzakwera; pakuti inacita zazikuru.
21 Usaopa, dziko iwe; kondwera, nusekerere; pakuti Yehova wacita zazikuru.
22 Musamaopa, nyama za kuthengo inu; pakuti m'cipululu muphukanso msipu; pakuti mitengo ibala zipatso zao; mikuyu ndi mipesa ipatsa mphamvu zao.
23 Mukondwere tsono, inu ana a Ziyoni, nimusekerere m'Yehova Mulungu wanu; pakuti adzayamba kukupatsani mvula yamyundo, monga mwa cilungamo cace; nakubvumbitsirani mvula, mvula yamyundo ndi yamasika mwezi woyamba.
24 Ndipo madwale adzakhala ndi tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta; zidzasefuka m'zosungiramo zao.
25 Ndipo ndidzakubwezerani zaka zidazidya dzombe, ndi cirimamine, ndi anoni, ndi cimbalanga, gulu langa lalikuru la nkhondo, limene ndinalitumiza pakati pa inu.
26 Ndipo mudzadyaidya ndi kukhuta, nimudzalemekeza dzina la Yehova Mulungu wanu, amene anacita nanu modabwiza; ndi anthu anga sadzacita manyazi nthawi zonse.
27 Ndipo mudzadziwa kuti Ine ndiri pakati pa Israyeli, ndi kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, palibe wina; ndi anthu anga sadzacita manyazi nthawi zonse.
28 Ndipo kudzacitika m'tsogolo mwace, ndidzatsanulira mzimu wanga pa anthu onse, ndi ana anu amuna ndi akazi adzanenera, akulu akulu anu adzalota maloto, anyamata anu adzaona masomphenya;
29 ndi pa akapolo ndi adzakazi omwe ndidzatsanulira mzimu wanga masiku awo.
30 Ndipo ndidzaonetsa zodabwiza kuthambo ndi pa dziko lapansi, mwazi, ndi moto, ndi utsi tolo.
31 Dzuwa lidzasanduka mdima, ndi mwezi udzasanduka mwazi, lisanadze tsiku la Yehova lalikuru ndi loopsa.
32 Ndipo kudzacitika kuti ali yense adzaitana pa dzina la Yehova adzapulumutsidwa; pakuti m'phiri la Ziyoni ndi m'Yerusalemu mudzakhala cipulumutso, monga Yehova anatero, ndi mwa otsala amene Yehova adzawaitana.
1 Pakuti taonani, masiku awo, ndi nthawi iyo, pamene ndibwera nao andende a Yuda ndi a Yerusalemu,
2 ndidzasonkhanitsa amitundu onse, ndi kutsikira nao ku cigwa ca Yosafati; ndipo ndidzaweruzana nao komweko za anthu anga, ndi colowa canga Israyeli, amene anawabalalitsa mwa amitundu, nagawa dziko langa,
3 Ndipo anacitira anthu anga maere, napereka mwana wamwamuna kusinthana ndi mkazi wadama, nagula vinyo ndi mwana wamkazi kuti amwe.
4 Ndiponso ndiri ndi ciani ndi inu, Turo ndi Zidoni, ndi malire onse a Afilisti? mudzandibwezera cilango kodi? Mukandibwezera cilango msanga, mofulumira, ndidzabwezera cilango canu pamutu panu,
5 Popeza inu munatenga siliva wanga ndi golidi wanga, ndi kulonga zofunika zanga zokoma m'akacisi anu;
6 munagulitsanso ana a Yuda ndi ana a Yerusalemu kwa ana a Yavani, kuwacotsa kutali kwa malire ao;
7 taonani, ndidzawautsa kumalo kumene munawagulitsako, ndi kubwezera cilango canu pamutu panu;
8 ndipo ndidzagulitsa ana ako amuna ndi akazi m'dzanja la ana a Yuda; ndipo iwo adzawagulitsa kwa anthu a Seba, kwa anthu okhala kutari; pakuti Yehova wanena.
9 Mulalikire ici mwa amitundu mukonzeretu nkhondo; utsani amuna amphamvu; amuna onse a nkhondo ayandikire nakwere.
10 Sulani makasu anu akhale malupanga, ndi anangwape anu akhale nthungo; wofoka anene, Ndine wamphamvu.
11 Fulumirani, idzani, amitundu inu nonse pozungulirapo; sonkhanani pamodzi, mutsitsire komweko amphamvu anu, Yehova.
12 Agalamuke amitundu, nakwerere ku cigwa ca Yosafati; pakuti ndidzakhala komweko kuweruza amitundu onse ozungulira,
13 Longani zenga, pakuti dzinthu dzaca; idzani, pondani, pakuti cadzala coponderamo mphesa; zosungiramo zisefuka; pakuti zoipa zao nzazikuru.
14 Aunyinji, aunyinji m'cigwa cotsirizira mlandu! pakuti layandikira tsiku la Yehova m'cigwacotsiriziramlandu.
15 Dzuwa ndi mwezi zada, ndi nyenyezi zibweza kuwala kwao.
16 Ndipo Yehova adzadzuma ali ku Ziyoni, ndi kumveketsa mau ace ali ku Yerusalemu; ndi thambo ndi dziko lapansi zidzagwedezeka; koma Yehova adzakhala copulumukirako anthu ace, ndi linga la ana a Israyeli.
17 Momwemo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu wakukhala m'Ziyoni, phiri langa lopatulika; pamenepo Yerusalemu adzakhala wopatulika, osapitanso alendo pakati pace,
18 Ndipo kudzacitika tsiku ilo mapiri adzakhetsa vinyo wozuna, ndi pazitunda padzayenda mkaka, ndi m'mitsinje yonse ya Yuda mudzayenda madzi; ndi madzi a kasupe adzaturuka m'nyumba ya Yehova, nadzamwetsa madzi cigwa ca Sitimu.
19 Aigupto adzasanduka bwinja, ndi Edomu adzasanduka cipululu copanda kanthu, cifukwa ca ciwawaci anawacitira ana a Yuda; popeza anakhetsa mwazi wosacimwa m'dziko lao.
20 Koma Yuda adzakhala cikhalire, ndi Yerusalemu ku mibadwo mibadwo.
21 Ndipo ndidzayeretsa mwazi wao umene sindinauyeretsa, pakuti Yehova akhala m'Ziyoni.