1

1 CAKA coyamba tsono ca Koresi mfumu ya ku Perisiya, kuti akwaniridwe mau a Yehova m'kamwa mwa Yeremiya, Yehova anautsa mzimu wa Koresi, kuti abukitse mau m'ufumu wace wonse, nawalembenso, ndi kuti,

2 Atero Koresi mfumu ya ku Perisiya, Yehova Mulungu Wam'mwamba anandipatsa maufumu onse a pa dziko lapansi, nandilangiza ndimmangire nyumba m'Yerusalemu, ndiwo m'Yuda.

3 Ali yense mwa inu a anthu ace onse, Mulungu wace akhale naye, akwere kumka ku Yerusalemu, ndiwo m'Yuda, nakaimange nyumba ya Yehova Mulungu wa Israyeli; Iye ndiye Mulungu wokhala m'Yerusalemu.

4 Ndipo ali yense wotsala pamalo pali ponse agonerapo iye, anthu a kumalo kwace amthandize ndi siliva, ndi golidi, ndi zoweta, ndi cuma, pamodzi ndi nsembe yaufulu ya kwa nyumba ya Mulungu iri ku Yerusalemu.

5 Pamenepo ananyamuka akulu a nyumba za makolo a Yuda ndi Benjamini, ndi ansembe, ndi Alevi, ndiwo onse amene Mulungu adawautsira mzimu wao akwere kukamanga nyumba ya Yehova iri ku Yerusalemu.

6 Ndipo onse akuwazinga analimbitsa manja ao ndi zipangizo za siliva, ndi golidi, ndi cuma, ndi zoweta, ndi zinthu za mtengo wace, pamodzi ndi nsembe zaufulu.

7 Koresi mfumu anaturutsanso zipangizo za nyumba ya Yehova, zimene Nebukadinezara adaziturutsa m'Yerusalemu, ndi kuziika m'nyumba ya milungu yace;

8 zomwezi Koresi mfumu ya ku Perisiya anaziturutsa ndi dzanja la Miteridati wosunga cumayo, naziwerengera Sezibazara kalonga wa Ayuda.

9 Kuwerenga kwace ndiko: mbizi zagolidi makumi atatu, mbizi zasiliva cikwi cimodzi, mipeni makumi awiri mphambu isanu ndi inai;

10 zikho zagolidi makumi atatu, zikho zasiliva zina mazana anai ndi khumi, zipangizo zina cikwi cimodzi.

11 Zipangizo zonse zagolidi ndi zasiliva ndizo zikwi zisanu ndi mazana anai. Izi zonse Sezibazara anakwera nazo, pokwera andende aja kucokera ku Babulo kumka ku Yerusalemu.

2

1 Ana a deralo, amene anakwera kuturuka m'ndende mwa andende aja Nebukadinezara mfumu ya Babulo adawatenga ndende kumka nao ku Babulo, nabwerera kumka ku Yerusalemu ndi Yuda, yense ku mudzi wace, ndi awa:

2 ndiwo amene adadza ndi Zerubabele, Yesuwa, Nehemiya, Seraya, Reelaya, Moredekai, Bilisani, Misipara, Bigivai, Rehumu, Baana. Kuwerenga kwa amuna a anthu a Israyeli ndiko:

3 ana a Parosi, zikwi ziwiri ndi zana limodzi mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.

4 Ana a Sefatiya, mazana atatu mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.

5 Ana a Ara, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi asanu ndi awiri kudza asanu.

6 Ana a Pahati Moabu, a ana a Yesuwa ndi Yoabu, zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi atatu kudza khumi ndi awiri.

7 Ana a Elamu, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi asanu ndi anai.

8 Ana a Zatu, mazana asanu ndi anai mphambu makumi anai kudza asanu.

9 Ana a Zakai, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi asanu ndi limodzi.

10 Ana a Bani, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi anai kudza awiri.

11 Ana a Bebai, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.

12 Ana a Asigadi, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi awiri ndi awiri.

13 Ana a Adonikamu, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi mmodzi.

14 Ana a Bigivai, zikwi ziwiri mphambu makumi asanu kudza asanu ndi mmodzi.

15 Ana a Adini, mazana anai mphambu makumi asanu kudza anai.

16 Ana a Ateri, a Hezekiya, makumi asanu ndi anai mphambu asanu ndi atatu.

17 Ana a Bezai, mazana atatu mphambu makumi awiri kudza atatu.

18 Ana a Yora, zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.

19 Ana a Hasumu, mazana awiri mphambu makumi awiri kudza atatu.

20 Ana a Gibara, makumi asanu ndi anai mphambu asanu.

21 Ana a Betelehemu zana limodzi mphambu makumi awiri kudza atatu.

22 Anthu a ku Netofa, makumi asanu mphambu asanu ndi mmodzi.

23 Anthu a ku Anatoti, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.

24 Ana a Azimaveti, makumi anai mphambu awiri.

25 Ana a Kiriyati Arimu, Kefira, ndi Beeroti, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi anai kudza atatu.

26 Ana a Rama ndi Gaba, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza mmodzi.

27 Anthu a Mikimasi, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.

28 Anthu a ku Beteli ndi Ai, mazana awiri mphambu makumi awiri kudza atatu.

29 Ana a Nebo, makumi asanu mphambu awiri.

30 Ana a Magabisi, zana limodzi mphambu makumi asanu kudza asanu ndi mmodzi.

31 Ana a Elamu wina, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi asanu ndi anai.

32 Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.

33 Ana a Lodi, Hadidi, ndi Ono, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi awiri kudza asanu.

34 Ana a Yeriko, mazana atatu mphambu makumi anai kudza asanu.

35 Ana a Senai, zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi limodzi kudza makumi atatu.

36 Ansembe: ana a Yedaya, a nyumba ya Yesuwa, mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu ndi awiri kudza atatu.

37 Ana a lmneri, cikwi cimodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.

38 Ana a Pasuru, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi anai ndi asanu ndi awiri.

39 Ana a Harimu, cikwi cimodzi mphambu khumi limodzi kudza asanu ndi awiri.

40 Alevi: ana a Yesuwa, ndi Kadimiyeli, ndiwo a ana a Hodariya, makumi asanu ndi awiri mphambu anai.

41 Oyimba: ana a Asafu, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.

42 Ana a odikira: ana a Sabumu, ana a Ateri, ana a Talimoni, ana a Akubu, ana a Hatita, ana a Sobai, onse pamodzi ndiwo zana limodzi mphambu makumi atatu kudza asanu ndi anai.

43 Anetini: ana a Ziha, ana a Hasufa, ana a Tabaoti,

44 ana a Kerosi, ana a Siaha, ana a Padoni,

45 ana a Lebano, ana a Hagaba, ana a Akubu,

46 ana a Hagabu, ana a Salimai, ana a Hanani,

47 ana a Gideli, ana a Gahari, ana a Reaya,

48 ana a Rezini, ana a Nekoda, ana a Gazamu,

49 ana a Uza, ana a Paseya, ana a Besai,

50 ana a Asina, ana a Mehunimu, ana a Nefusimu,

51 ana a Bakabuku, ana a Hakufa, ana a Haruri,

52 ana a Baziluti, ana a Mehida, ana a Harisa,

53 ana a Barikosi, ana a Siseri, ana a Tama,

54 ana a Neziya, ana a Hatifa.

55 Ana a akapolo a Solomo: ana a Sotai, ana a Sofereti, ana a Peruda,

56 ana a Yaala, ana a Darikoni, ana a Gideli,

57 ana a Sefatiya, ana a Hatili, ana a Pokereti wa Zebaimu, ana a Ami.

58 Anetini onse, ndi ana a akapolo a Solomo, ndiwo mazana atatu mphambu makumi asanu ndi anai kudza awiri.

59 Ndipo okwera kucokera ku Telemela, Teleharisa, Kerubi, Adana, Imeri, ndi awa, koma sanakhoza kuchula nyumba za makolo ao ndi mbumba zao ngati ali Aisrayeli:

60 ana a Delaya, ana a Tobiya, ana a Nekoda, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.

61 Ndi ana a ansembe: ana a Habaya, ana a Kozi, ana a Barizilai, amene anadzitengera mkazi wa ana akazi a Barizilai Mgileadi, nachedwa dzina lao.

62 Awa anafunafuna maina ao m'buku la iwo owerengedwa mwa cibadwidwe cao, koma osawapeza; potero anacotsedwa ku nchito ya nsembe monga odetsedwa.

63 Ndipo kazembe anawauza kuti asadyeko zopatulikitsa, mpaka adzabuka wansembe wokhala ndi Urimu ndi Tumimu.

64 Msonkhano wonse pamodzi ndiwo wa zikwi makumi anai ndi awiri mphambu mazana atatu kudza makumi asanu ndi limodzi,

65 osawerenga akapolo ao amuna ndi akazi, ndiwo zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu mazana atatu ndi makumi atatu kudza asanu ndi awiri; ndipo anakhala nao amuna ndi akazi oyimbira mazana awiri.

66 Akavalo ao ndiwo mazana asanu ndi awiri mphambu makumi atatu kudza asanu ndi mmodzi; nyuru zao mazana awiri mphambu makumi anai kudza zisanu;

67 ngamira zao mazana anai mphambu makumi atatu kudza asanu; aburu zikwi zisanu ndi cimodzi mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi awiri.

68 Ndipo akulu ena a nyumba za makolo, pofika ku nyumba ya Yehova iri ku Yerusalemu, anapereka caufulu kwa nyumba ya Mulungu cakulimika pakuzika pace.

69 Monga momwe anakhoza anapereka ku cuma ca nchitoyi madariki agolidi: zikwi zisanu ndi cimodzi, miyeso ya siliva zikwi zisanu, ndi maraya a ansembe zana limodzi.

70 Ndipo ansembe, ndi Alevi, ndi anthu ena, ndi oyimbira, ndi odikira, ndi Anetini, anakhala m'midzi mwao, ndi Aisrayeli onse m'midzi mwao.

3

1 Utakhala tsono mwezi wacisanu ndi ciwiri, ana a Israyeli ali m'midzimo, anthuwo anasonkhana ngati munthu mmodzi ku Yerusalemu.

2 Nanyamuka Yesuwa mwana wa Yozadaki, ndi abale ace ansembe, ndi Zerubabele mwana wa Sealitiyeli, ndi abale ace, namanga guwa la nsembe la Mulungu wa Israyeli, kuperekapo nsembe zopsereza, monga mulembedwa m'cilamulo ca Mose munthu wa Mulungu.

3 Ndipo anakhazika guwa la nsembe patsinde pace cifukwa ca kuopa iwo anthu a m'maikomo; nakwezera Yehova nsembe zopsereza pamenepo, nsembe zopsereza zam'mawa ndi zamadzulo.

4 Nacita madyerero a misasa monga kwalembedwa, napereka nsembe yopsereza tsiku ndi tsiku mawerengedwe ace, monga mwa lamulo lace la tsiku lace pa tsiku lace;

5 atatero anaperekanso nsembe yopsereza yosalekeza, ndi za pokhala mwezi, ndi za nyengo zoikika zonse za Yehova zopatulika, ndi za munthu yense wopereka nsembe yaufulu kwa Yehova mwaufulu.

6 Ciyambire tsiku loyamba la mwezi wacisanu ndi ciwiri anapereka nsembe zopsereza kwa Yehova; koma sanamange maziko a Kacisi wa Yehova.

7 Anaperekanso ndarama kwa amisiri a miyala, ndi a mitengo; ndi cakudya, ndi cakumwa, ndi mafuta, kwa a ku Sidoni, ndi a ku Turo, kuti atenge mikungudza ku Lebano, kufika nayo ku nyanja ku Yopa, monga adawalola Koresi mfumu ya Babulo.

8 Caka caciwiri tsono cakufika iwo ku nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu, mwezi waciwiri, Zerubabele mwana wa Sealitiyeli, ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki, ndi abale ao otsala, ansembe ndi Alevi ndi onse ocokera kundende kudza ku Yerusalemu, anayamba, naika Alevi a zaka makumi awiri ndi mphambu, ayang'anire nchito ya nyumba ya Yehova.

9 Pamenepo anaimirira pamodzi Yesuwa ndi ana ace ndi abale ace, Kadimiyeli ndi ana ace, ana a Yuda, kuyang'anira ogwira nchito m'nyumba ya Yehova, ana a Henadadi ndi ana ao ndi abale ao Alevi.

10 Ndipo pomanga maziko a Kacisi wa Yehova, amisiriwo anaimiritsa ansembe obvala zobvala zao ndi mphalasa, ndi Alevi ana a Asafu ndi nsanje, kuti alemekeze Yehova, monga umo anaikiratu Davide mfumu ya Israyeli.

11 Ndipo anathirirana mang'ombe, kulemekeza ndi kuyamika Yehova, ndi kuti, Pakuti ndiye wabwino, pakuti cifundo cace ncosalekeza pa Israyeli. Napfuula anthu onse ndi cipfuu cacikuru, pomlemekeza Yehova; popeza adamanga maziko a nyumba ya Yehova.

12 Koma ansembe ambiri, ndi Alevi, ndi akuru a nyumba za makolo, okalamba amene adaona nyumba yoyamba ija, pomanga maziko a nyumba iyi pamaso pao, analira ndi mau akuru; koma ambiri anapfuulitsa mokondwera.

13 Potero anthu sanazindikira phokoso la kupfuula mokondwera kulisiyanitsa ndi phokoso la kulira kwa anthu; pakuti anthu anapfuulitsa kwakukuru, ndi phokoso lace lidamveka kutari.

4

1 Atamva tsono a adani Yuda ndi Benjamini kuti ana aja a ndende analikumangira Yehova Mulungu wa Israyeli Kacisi,

2 anayandikira kwa Zerubabele, ndi kwa akulu a nyumba za makolo, nanena nao, Timange pamodzi nanu; pakuti timfuna Mulungu wanu monga inu, ndipo timamphera nsembe ciyambire masiku a Ezaradoni mfumu ya Asuri, amene anatikweretsa kuno.

3 Koma Zerubabele, ndi Yesuwa, ndi akuru otsala a nyumba za makolo a Israyeli, anati kwa iwo, Sikuyenera ndi inu ndi ife kumangira Mulungu wathu nyumba, koma ife tokha pamodzi tidzamangira Yehova Mulungu wa Israyeli, monga mfumu Koresi mfumu ya Perisiya watilamulira.

4 Pamenepo anthu a m'dziko anafoketsa manja a anthu Ayuda, nawabvuta pomanga,

5 nalembera opangira atsutsane nao, nafafanize uphungu wao, masiku onse a Koresi mfumu ya Perisiya, mpaka ufumu wa Dariyo mfumu ya Perisiya.

6 Ndipo pokhala mfumu Ahaswero, poyambira ufumu wace, analembera cowaneneza okhala m'Yuda ndi m'Yerusalemu.

7 Ndipo masiku a Aritasasta Bisilamu, Mitiredati, Tabeeli, ndi anzao otsala, analembera kwa Aritasasta mfumu ya Perisiya; ndi cilembedwe cace ca kalatayo anamlemba m'Ciaramu, namsanduliza m'Ciaramu.

8 Rehumu ciwinda ca malamulo, ndi Simsai mlembi, analemba kalata kwa mfumu Aritasasta, wakutsutsana naye Yerusalemu motere:

9 nalembera Rehumu ciwinda ca malamulo, ndi Simsai mlembi, ndi anzace otsala; Adinai, ndi Afarisatikai, Ataripilai, Afarisai, Arekavai, Ababulo, Asusanekai, Adehai, Aelimai,

10 ndi amitundu otsala amene, Osinapera wamkuru ndi womveka adawatenga mikoli, nawakhalitsa m'mudzi wa Samariya, ndi m'dziko lotsala tsidya lino la mtsinje wa Firate, pa nthawi yakuti.

11 Zolembedwa m'kalatayo anamtumiza kwa Aritasasta mfumu ndizo: Akapolo anu, anthu a tsidya lino la mtsinjewo, ndi pa nthawi yakuti.

12 Adziwe mfumu kuti, Ayuda adakwerawo ocokera kwanu atifikira ife ku Yerusalemu, alikumanga mudzi uja wopanduka ndi woipa, alikutsiriza malinga ace, nalumikiza maziko ace.

13 Adziwe tsono mfumu, kuti akamanga mudzi uwu ndi kutsiriza malinga ace, sadzapereka msonkho, kapena thangata, kapena msonkho wa m'njira; ndipo potsiriza pace kudzasowetsa mafumu.

14 Popeza tsono timadya mcere wa m'nyumba ya mfumu, sitiyenera kungopenyerera mpepulo wa pa mfumu; cifukwa cace tatumiza ndi kudziwitsa mfumu,

15 kuti afunefune m'buku la cikumbutso la makolo anu; momwemo mudzapeza m'buku la cikumbutso, ndi kudziwa kuti mudzi uwu ndi mudzi wopanduka, ndi wosowetsa mafumu, ndi maiko; ndi kuti amadziyendera m'menemo kuyambira kale lomwe; ndico cifukwa cakuti anapasula mudzi uwu.

16 Tirikudziwitsa mfumu kuti ukamangidwa mudziwu, nakatsirizidwa malinga ace, simudzakhala nalo gawo tsidya lino la mtsinjewo.

17 Mfumu nibweza mau kwa Rehumu ciwinda ca malamulo, ndi kwa Simsai mlembi, ndi kwa anzao otsala okhala m'Samariya, ndi otsala tsidya lino la mtsinjewo, Mtendere, ndi nthawi yakuti.

18 Kalatayo mwatitumizira anandiwerengera momveka.

19 Ndipo ndinalamulira anthu, nafunafuna, napeza kuti mudzi uwu unaukira mafumu kuyambira kale lomwe ndi kuti akacitamo mpanduko ndi kudziyendera.

20 Panalinso mafumu amphamvu m'Yerusalemu amene anacita ufumu tsidya lija lonse la mtsinje, ndipo anthu anawapatsa msonkho, thangata, ndi msonkho wa m'njira.

21 Mulamulire tsono kuti anthu awa aleke, ndi kuti asamange mudzi uwu, mpaka ndidzalamulira ndine.

22 Cenjerani mungadodomepo, cidzakuliranji cisauko ca kusowetsa mafumu?

23 Pamenepo atawerenga malemba a kalata wa mfumu kwa Rehumu, ndi Simsai mlembi, ndi anzao, anafulumira kupita ku Yerusalemu kwa Ayuda, nawaletsa ndi dzanja lamphamvu.

24 Momwemo inalekeka nchito ya nyumba ya Mulungu yokhala ku Yerusalemu; nilekeka mpaka caka caciwiri ca ufumu wa Dariyo mfumu ya Perisiya.

5

1 Ndipo aneneri, Hagai mneneriyo, ndi Zekariya mwana wa Ido, ananenera kwa Ayuda okhala m'Yuda ndi m'Yerusalemu; m'dzina la Mulungu wa Israyeli ananenera kwa iwo.

2 Pamenepo Zerubabele mwana wa Sealitiyeli, ndi Yesuwa mwana wa Yozadaki, ananyamuka, nayamba kumanga nyumba ya Mulungu iri ku Yerusalemu, anali pamodzi nao aneneri a Mulungu akuwathandiza.

3 Nthawi yomweyi anawadzera Tatinai kazembe tsidya lino la mtsinjewo, ndi Setara Bozinai, ndi anzao, nanena nao motere, Anakulamulirani inu ndani kumanga nyumba iyi, ndi kutsiriza khoma ili?

4 Nanena naonso motere, Maina ao a anthu omanga cimangidwe ici ndiwo ayani?

5 Koma diso la Mulungu wao linali pa akuru a Ayuda, ndipo sanawaletsa mpaka mlandu unamdzera Dariyo, nabweza mau a mlanduwo m'kalata.

6 Zolembedwa m'kalata amene Tatinai kazembe wa tsidya lino la mtsinjewo, ndi Setara Bozenai, ndi anzace Afarisikai, okhala tsidya lino la mtsinje, anatumiza kwa Dariyo mfumu,

7 anatumiza kalata kwa iyeyo m'menemo munalembedwa motere, Kwa Dariyo mfumu, mtendere wonse.

8 Adziwe mfumu kuti ife tinamuka ku dziko la Yuda, ku nyumba ya Mulungu wamkuru, yomangidwa ndi miyala yaikuru, niikidwa mitengo pamakoma, nicitika mofulumira nchitoyi, nikula m'dzanja mwao.

9 Pamenepo tinafunsa akulu aja ndi kutere nao, Anakulamulirani ndani kumanga nyumba iyi, ndi kutsiriza khoma ili?

10 Tinawafunsanso maina ao, kukudziwitsani, kuti tilembere maina a anthu akuwatsogolera.

11 Natiyankha mau motere, ndi kuti, Ife ndife akapolo a Mulungu wa Kumwamba ndi dziko lapansi, tirikumanga nyumba imene idamangika zapita zaka zambiri; inaimanga ndi kuitsiriza mfumu yaikuru ya Israyeli.

12 Koma makolo athuwo atautsa mkwiyo wa Mulungu wa Kumwamba, Iye anawapereka m'dzanja la Nebukadinezara mfumu ya ku Babulo Mkasidi, amene anaononga nyumba yino, natenga anthu ndende kumka nao ku Babulo.

13 Koma caka coyamba ca Koresi mfumu ya Babulo, Koresi mfumuyo analamulira kuti azimanga nyumba iyi ya Mulungu.

14 Ndiponso zipangizo za golidi ndi siliva za nyumba ya Mulungu, anaziturutsa Nebukadinezara m'Kacisi anali ku Yerusalemu, ndi kubwera nazo ku kacisi wa ku Babulo, izizo Koresi mfumu anaziturutsa m'kacisi wa ku Babulo, nazipereka kwa munthu dzina lace Sezibazara, amene anamuika akhale kazembe;

15 nati naye, Tenga zipangizo izi, kaziike m'Kacisi ali m'Yerusalemu, nimangidwe nyumba ya Mulungu pambuto pace.

16 Pamenepo anadza Sezibazara yemweyo namanga maziko a nyumba ya Mulungu iri m'Yerusalemu; ndipo kuyambira pomwepo kufikira tsopano irimkumangidwa, koma siinatsirizike.

17 Ndipo tsono cikakomera mfumu, munthu asanthule m'nyumba ya cuma ca mfumu iri komwe ku Babulo, ngati nkuterodi, kuti Koresi mfumu analamulira kuti azimanga nyumba iyi ya Mulungu ku Yerusalemu; ndipo mfumu ititumizire mau omkomera pa cinthuci.

6

1 Pamenepo analamulira Dariyo mfumu, ndipo anthu anafunafuna m'nyumba ya mabuku mosungira cuma m'Babulo.

2 Napeza ku Akimeta m'nyumba ya mfumu m'dera la Mediya, mpukutu, ndi m'menemo munalembedwa motere, cikhale cikumbutso:

3 Caka coyamba ca Koresi mfumu, analamulira Koresi mfumuyo, Kunena za nyumba ya Mulungu ku Yerusalemu, imangidwe nyumbayi pamalo pophera nsembe, namangidwe kolimba maziko ace, msinkhu wace mikono makumi asanu ndi limodzi, kupingasa kwace mikono makumi asanu ndi limodzi;

4 ndi mipambo itatu ya miyala yaikuru, ndi mpambo wa mitengo yatsopano; nalipidwe ndarama zocokera ku nyumba ya mfumu.

5 Ndi zipangizo za golidi ndi siliva za nyumba ya Mulungu, zimene anaziturutsa Nebukadinezara m'Kacisi ali ku Yerusalemu, nazitenga kumka nazo ku Babulo, azibwezere, nabwere nazo ku Kacisi ali ku Yerusalemu, ciri conse ku malo ace; naziike m'nyumba ya Mulungu.

6 Tsono iwe, Tatinai, kazembe wa tsidya lija la mtsinjewo, Setara Bozenai, ndi anzanu Afarisikai, okhala tsidya lija la mtsinje, muzikhala kutali;

7 lekani nchito iyi ya Mulungu, osaibvuta; kazembe wa Ayuda ndi akulu a Ayuda amange nyumba iyi ya Mulungu pambuto pace.

8 Ndilamuliranso za ici muzicitira akuru awa a Ayuda, kuti amange nyumba iyi ya Mulungu, ndiko kuti mutengeko cuma ca mfumu, ndico msonkho wa tsidya la mtsinje, nimupereke zolipira kwa anthu awa msanga, angawacedwetse.

9 Ndipo zosowa zao, ana a ng'ombe, ndi nkhosa zamphongo, ndi ana a nkhosa, zikhale nsembe zopsereza za Mulungu wa Kumwamba; tirigu, mcere, vinyo, mafuta, monga umo adzanena ansembe ali ku Yerusalemu, ziperekedwe kwa iwo tsiku ndi tsiku, zisasoweke;

10 kuti apereke nsembe zonunkhira bwino kwa Mulungu wa Kumwamba, napempherere moyo wa mfumu ndi wa ana ace.

11 Ndalamuliranso kuti ali yense adzasintha mau awa, usololedwe mtanda kunyumba kwace, namkweze, nampacike pomwepo; niyesedwe dzala nyumba yace cifukwa ca ici;

12 ndipo Mulungu wokhalitsa dzina lace komweko agwetse mafwnu onse ndi mitundu yonse ya anthu, akuturutsa dzanja lao kusintha mau awa, kuononga nyumba ya Mulungu iri ku Yerusalemu. Ine Dariyo ndalamulira, cicitike msanga.

13 Pamenepo Tatinai kazembe wa tsidya lino la mtsinjewo, Setara Bozenai, ndi anzao, popeza mfumu Dariyo adatumiza mau, anacita momwemo cofulumira.

14 Ndipo akulu a Ayuda anamanga opanda cosoweka, mwa kunenera kwa mneneri Hagai, ndi Zekariya mwana wa Ido. Naimanga, naitsiriza, monga mwa lamulo la Mulungu wa Israyeli, ndi monga mwa lamulo la Koresi, ndi Dariyo, ndi Aritasasta mfumu ya Perisiya,

15 Nitsirizidwa nyumba iyi tsiku lacitatu la mwezi wa Adara, ndico caka cacisanu ndi cimodzi ca ufumu wa Dariyo mfumu.

16 Ndipo ana a Israyeli, ansembe ndi Alevi, ndi ana otsala a ndende, anapereka nyumba iyi ya Mulungu mokondwera.

17 Ndipo popatulira nyumba iyi ya Mulungu anapereka ng'ombe zana limodzi, nkhosa zamphongo mazana awiri, ana a nkhosa mazana anai, ndi za nsembe yazolakwa ya Aisrayeli onse atonde khumi ndi awiri, monga mwa kuwerenga kwace kwa mapfuko a Israyeli.

18 Naika ansembe m'magawo mwao, ndi Alevi m'magawidwe mwao, atumikire Mulungu wokhala ku Yerusalemu, monga mulembedwa m'buku la Mose.

19 Ndipo ana a ndende anacita Paskha tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi woyamba.

20 Pakuti ansembe ndi Alevi anadziyeretsa pamodzi, anayera onsewo, naphera Paskha cifukwa ca ana onse a ndende, ndi abale ao ansembe, ndi iwo okha.

21 Ndipo ana a Israyeli obwera kundende, ndi yense wakudzipatulira kucokera conyansa ca amitundu, kutsata iwowa, kufuna Yehova Mulungu wa Israyeli, anadza,

22 nasunga madyerero a mkate wopanda cotupitsa masiku asanu ndi awiri ndi cimwemwe; pakuti Yehova adawakondweretsa, nawatembenuzira mtima wa mfumu ya Asuri, kulimbitsa manja ao mu nchito ya nyumba ya Mulungu, Mulungu wa Israyeli.

7

1 Zitatha izi tsono, pokhala mfumu Aritasasta mfumu ya Perisiya, anadza Ezara mwana wa Seraya, mwana wa Azariya, mwana wa Hilikiya,

2 mwana wa Salumu, mwana wa Zadoki, mwana wa Ahitubu,

3 mwana wa Amariya, mwana wa Azariya, mwana wa Meraioti,

4 mwana wa Zerahiya, mwana wa Uzi, mwana wa Buki,

5 mwana wa Abisuwa mwana wa Pinehasi, mwana wa Eleazara, mwana wa Aroni wansembe wamkuru.

6 Ezara amene anakwera kucokera ku Babulo, ndiye mlembi waluntha m'cilamulo ca Mose, cimene Yehova Mulungu wa Israyeli adacipereka; ndipo mfumu inampatsa copempha iye conse, monga linamkhalira dzanja la Yehova Mulungu wace.

7 Nakweranso kumka ku Yerusalemu ena a ana a Israyeli, ndi ansembe, ndi Alevi, ndi oyimbira, ndi odikira, ndi Anetini, caka cacisanu ndi ciwiri ca Aritasasta mfumu.

8 Ndipo iye anafika ku Yerusalemu mwezi wacisanu, ndico caka cacisanu ndi ciwiri ca mfumu.

9 Pakuti tsiku loyamba la mwezi woyamba, ndilo ciyambi ca ulendo wokwera kucokera ku Babulo, ndi tsiku lacimodzi la mwezi wacisanu anafika ku Yerusalemu, monga linamkhalira dzanja lokoma la Mulungu wace.

10 Pakuti Ezara adaikiratu mtima wace kucifuna cilamulo ca Yehova, ndi kucicita, ndi kuphunzitsa m'Israyeli malemba ndi maweruzo.

11 Malemba a kalatayo mfumu Aritasasta anampatsa Ezara wansembe mlembi, ndiye mlembi wa mau a malamulo a Yehova, ndi malemba ace kwa Israyeli, ndi awa:

12 Aritasasta mfumu ya mafumu kwa Ezara wansembe, mlembi wa lamulo la Mulungu wa Kumwamba, mtendere weni weni, ndi pa nthawi yakuti.

13 Ndilamulira kuti onse a ana a Israyeli, ndi ansembe ao, ndi Alevi, m'ufumu wanga, ofuna eni ace kumuka ku Yerusalemu, apite nawe.

14 Popeza utumidwa wocokera pamaso pa mfumu ndi aphungu ace asanu ndi awiri, kufunsira za Yuda ndi Yerusalemu monga mwa lamulo la Mulungu wako liri m'dzanja lako,

15 ndi kumuka nazo siliva ndi golidi, zimene mfumu ndi aphungu ace, anapereka mwaufulu kwa Mulungu wa Israyeli, mokhala mwace muli m'Yerusalemu,

16 pamodzi ndi siliva ndi golidi ziri zonse ukazipeza m'dziko lonse la ku Babulo, pamodzi ndi copereka caufulu ca anthu, ndi ca ansembe, akuperekera mwaufulu nyumba ya Mulungu wao iri ku Yerusalemu;

17 m'mwemo uzifulumira kugula ndi ndalama iyi ng'ombe, nkhosa zamphongo, ana a nkhosa, pamodzi ndi nsembe zao zaufa, ndi nsembe zao zothira; ndi kuzipereka pa guwa la nsembe la nyumba ya Mulungu wanu yokhala ku Yerusalemu.

18 Ndipo ciri conse cidzakomera iwe ndi abale ako kucita nazo siliva ndi golidi zotsala, ici mucite monga mwa cifuniro ca Mulungu wanu.

19 Ndipo zipangizozo akupatsa za utumiki wa nyumba ya Mulungu wako, uzipereka pamaso pa Mulungu wa ku Yerusalemu.

20 Ndi zina zotsala zakusowa nyumba ya Mulungu wako, zikayenera uzipereke, uzipereke zocokera ku nyumba ya cuma ca mfumu.

21 Ndipo ine Aritasasta, mfumu ine, ndilamulira osunga cuma onse okhala tsidya lija la mtsinjewo, kuti ciri conse akupemphani Ezara wansembe, mlembi wa lamulo la Mulungu wa Kumwamba, cicitike mofulumira;

22 mpaka matalente a siliva zana limodzi, ndi miyeso ya tirigu zana limodzi, ndi miyeso ya vinyo zana limodzi, ndi miyeso ya mafuta zana limodzi, ndi mcere wosauwerenga.

23 Ciri conse Mulungu wa Kumwamba acilamulire cicitikire mwacangu nyumba ya Mulungu wa Kumwamba; pakuti padzakhaliranji mkwiyo pa ufumu wa mfumu ndi ana ace?

24 Tikudziwitsaninso kuti sikudzaloledwa kusonkhetsa ali yense wa ansembe, ndi Alevi, oyimbira, odikira, Anetini, kapena anchito a nyumba iyi ya Mulungu msonkho, thangata, kapena msonkho wa panjira.

25 Ndipo iwe Ezara monga mwa nzeru za Mulungu wako iri m'dzanja lako, uike nduna, ndi oweruza mirandu, aweruze anthu onse ali tsidya lija la mtsinje, onse akudziwa malamulo a Mulungu wako; ndi wosawadziwayo umphunzitse.

26 Ndipo ali yense wosacita lamulo la Mulungu wako, ndi lamulo la mfumu, mlandu umtsutse msanga, ngakhale kumupha, kapena kumpitikitsa m'dziko, kapena kumlanda cuma cace, kapena kummanga m'kaidi.

27 Wodala Yehova Mulungu wa makolo athu, amene anaika cinthu cotere mu mtima wa mfumu, kukometsera nyumba ya Yehova iri ku Yerusalemu,

28 nandifikitsira cifundo pamaso pa mfumu, ndi aphungu ace, ndi pamaso pa akalonga amphamvu onse a mfumu. Motero ndinalimbika mtima, monga umo dzanja la Yehova Mulungu wanga linakhala pa ine; ndipo ndinasonkhanitsa mwa Israyeli anthu omveka akwere nane limodzi.

8

1 Ndipo akuru a nyumba za makolo ndi awa, ndi cibadwidwe ca iwo okwera nane limodzi kucokera ku Babulo, pokhala mfumu Aritasasta, ndi ici:

2 wa ana a Pinehasi, Gerisomu; wa ana a Itamara, Danieli; wa ana a Davide, Hatusi.

3 Wa ana a Sekaniya, wa ana a Parosi, Zekariya; ndi pamodzi naye, powawerenga monga mwa cibadwidwe cao, amuna zana limodzi mphambu makumi asanu.

4 Wa ana a Pahati Moabu, Elihoenai mwana wa Zerahiya; ndi pamodzi naye amuna mazana awiri.

5 Wa ana a Sekaniya, mwana wa Yahazieli; ndi pamodzi naye amuna mazana atatu.

6 Ndi wa ana a Adini, Ebedi mwana wa Yonatani; ndi pamodzi naye amuna makumi asanu.

7 Ndi wa ana a Elamu, Yesaya mwana wa Ataliya; ndi pamodzi naye amuna makumi asanu ndi awiri.

8 Ndi wa ana a Sefatiya, Zebadiya mwana wa Mikaeli; ndi pamodzi naye amuna makumi asanu ndi atatu.

9 Wa ana a Yoabu, Obadiya mwana wa Yehieli; ndi pamodzi naye amuna mazana awiri mphambu khumi kudza asanu ndi atatu.

10 Ndi wa ana a Selomiti, mwana wa Yosifiya; ndi pamodzi naye amuna zana limodzi mphambu makumi asanu ndi limodzi.

11 Ndi wa ana a Bebai, Zekariya mwana wa Bebai; ndi pamodzi naye amuna makumi awiri mphambu asanu ndi atatu.

12 Ndi wa ana a Azigadi, Yohanana mwana wa Hakatana; ndi pamodzi naye amuna zana limodzi mphambu khumi limodzi.

13 Ndi a ana otsiriza a Adonikmnu, maina ao ndiwo Elifeleti, Yeueli, ndi Semaya; ndi pamodzi nao amuna makumi asanu ndi limodzi.

14 Ndi wa ana a Bigivai, Utai ndi Zabudi, ndi pamodzi nao amuna makumi asanu ndi awiri.

15 Ndipo ndinawasonkhanitsa ku mtsinje wopita ku Ahava, ndi komweko tinakhala m'misasa masiku atatu; ndipo ndinapenyerera anthu ndi ansembe, koma sindinapezapo wa ana a Levi.

16 Pamenepo ndinatumiza munthu kuitana Eliezere, Ariyeli, Semaya, ndi Elimatana, ndi Natani, ndi Zekariya, ndi Mesulamu, ndiwo akuru; ndi Yoyaribi ndi Elinatani, ndiwo aphunzitsi.

17 Ndipo ndinawatumiza kwa Ido mkuru, ku malo dzina lace Kasifiya; ndinalooganso m'kamwa mwao mau akunena kwa Ido, ndi kwa abale ace Anetini, pa malo paja Kasifiya, kuti azibwera nao kwa ife otumikira za nyumba ya Mulungu wathu.

18 Ndipo monga munatikhalira dzanja lokoma la Mulungu wathu, anatitengera munthu wanzeru wa ana a Mali, mwana wa Levi, mwana wa Israyeli; ndi Serebiya, pamodzi ndi ana ace ndi abale ace khumi mphambu asanu ndi atatu;

19 ndi Hasabiya, ndi pamodzi naye Yesaya wa ana a Merari, abale ace ndi ana ao makumi awiri;

20 ndi a Anetini, amene Davide ndi akalonga adapereka atumikire Alevi, Anetini mazana awiri mphambu makumi awiri, onsewo ochulidwa maina.

21 Pamenepo ndinalalikira cosala komweko ku mtsinje wa Ahava, kuti tidzicepetse pamaso pa Mulungu wathu, kumfunsa ationetsere njira yolunjika ya kwa ife, ndi ang'ono athu, ndi cuma cathu conse.

22 Pakuti ndinacita manyazi kupempha kwa mfumu gulu la asilikari, ndi apakavalo, kutithandiza pa adani panjira; popeza tidalankhula ndi mfumu kuti, Dzanja la Mulungu wathu likhalira mokoma onse akumfuna; koma mphamvu yace ndi mkwiyo wace zitsutsana nao onse akumsiya.

23 Momwemo tinasala ndi kupempha ici kwa Mulungu wathu; natibvomereza Iye,

24 Pamenepo ndinapatula akulu a ansembe khumi ndi awiri, ndiwo Serebiya, Hasabiya, ndi abale ao khumi pamodzi nao,

25 ndi kuwayesera siliva, ndi golidi, ndi zipangizo, ndizo copereka ca kwa nyumba ya Mulungu wathu, cimene mfumu, ndi aphungu ace, ndi akalonga ace, ndi Aisrayeli onse anali apawa, adapereka.

26 Ndipo ndinawayesera m'dzanja mwao matalente a siliva mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu, ndi zipangizo zasiliva matalente zana limodzi,

27 ndi zikho zagolidi makumi awiri za madariki cikwi cimodzi, ndi zipangizo ziwiri za mkuwa wabwino wonyezimira wokhumbika ngati golidi.

28 Ndipo ndinanena nao, Inu ndinu opatulikira Yehova, ndi zipangizozo nzopatulikira, ndi siliva ndi golidi, ndizo copereka caufulu ca kwa Yehova Mulungu wa makolo anu.

29 Mukhale maso ndi kuzisunga mpaka muziyesera pamaso pa akulu a ansembe ndi Alevi, ndi akulu a nyumba za makolo a Israyeli ku Yerusalemu, m'zipinda za nyumba ya Yehova.

30 Potero ansembe ndi Alevi analandira kulemera kwace kwa siliva ndi golidi ndi zipangizo, abwere nazo ku Yerusalemu ku nyumba ya Mulungu wathu.

31 Pamenepo tinacoka ku mtsinje wa Ahava tsiku lakhumi ndi ciwiri la mwezi woyamba, kumka ku Yerusalemu; ndipo dzanja la Mulungu wathu linakhala pa ife, ndi kutilanditsa m'dzanja la mdani ndi wolalira m'njira.

32 Ndipo tinafika ku Yerusalemu ndi kukhalako masiku atatu.

33 Ndi pa tsiku lacinai siliva ndi golidi ndi zipangizo zinayesedwa m'nyumba ya Mulungu wathu, m'dzanja la Meremoti mwana wa Uliya wansembe, ndi pamodzi naye Eleazara mwana wa Pinehasi, ndi pamodzi nao Yozabadi mwana wa Yesuwa, ndi Nowadia mwana wa Binui, Alevi;

34 zonsezi anaziwerenga ndi kuziyesa; ndi kulemera kwace konse kunalembedwa nthawi yomweyo.

35 Otengedwa ndende, ataturuka m'ndende, anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu wa Israyeli, ng'ombe khumi ndi ziwiri za Aisrayeli onse, nkhosa zamphongo makumi asanu ndi anai mphambu zisanu ndi imodzi, ana a nkhosa makumi asanu ndi awiri mphambu asanu ndi awiri, atonde khumi ndi awiri, akhale nsembe yazolakwa; zonsezi ndizo nsembe yopsereza ya kwa Yehova.

36 Ndipo anapereka malamulo a mfumu kwa akazembe a mfumu, ndi kwa ziwanga, tsidya lino la mtsinjewo; ndipo iwo anathandiza anthu ndi nyumba ya Mulungu.

9

1 Zitatha izi tsono anandiyandikira akalonga, ndi kuti, Anthu a Israyeli, ndi ansembe, ndi Alevi, sanadzilekanitsa ndi anthu a maikowa, kunena za zonyansa zao za Akanani, Ahiti, Aperizi, Ayebusi, Aamoni, Amoabu, Aaigupto, ndi Aamori.

2 Pakuti anadzitengera okha ndi ana amuna ao ana akazi ao; nisokonezeka mbeu yopatulika ndi mitundu ya maikowa; inde dzanja la akalonga ndi olamulira linayamba kulakwa kumene.

3 Ndipo pakumva mau awa ndinang'amba cobvala canga, ndi maraya anga, ndi kumwetula tsitsi la pamutu panga ndi ndebvu zanga, ndi kukhala pansi m'kudabwa.

4 Nandisonkhanira ali yense wakunjenjemera pa mau a Mulungu wa Israyeli, cifukwa ca kulakwa kwa iwo a ndende; ndipo ndinakhala m'kudabwa mpaka nsembe yamadzulo.

5 Ndi pa nsembe yamadzulo ndinanyamuka m'kuzunzika kwanga, cobvala canga ndi maraya anga zong'ambika; ndipo ndinagwada ndi maondo anga, ndi kutambasula manja anga kwa Yehova Mulungu wanga;

6 ndipo ndinati, Mulungu wanga, ndigwa nkhope, ndi kucita manyazi kuweramutsa nkhope yanga kwa inu Mulungu wanga, popeza mphulupulu zathu zacuruka pamtu pathu, ndi kuparamula kwathu kwakula kufikira m'Mwamba.

7 Ciyambire masiku a makolo athu taparamula kwakukuru mpaka lero lino; ndi cifukwa ca mphulupulu zathu ife, mafumu athu, ndi ansembe athu, tinaperekedwa m'dzanja la mafumu a maikowo, kulupanga kundende, ndi kufunkhidwa, ndi kucitidwa manyazi pankhope pathu, monga lero lino.

8 Ndipo tsopano, kamphindi, Yehova Mulungu wathu wationetsa cisomo, kutisiyira cipulumutso, ndi kutipatsa ciciri m'malo mwace mopatulika; kuti Mulungu wathu atipenyetse m'maso mwathu, ndi kutitsitsimutsa pang'ono m'ukapolo wathu.

9 Popeza ife ndife akapolo, koma Mulungu wathu sanatisiya m'ukapolo wathu, natifikitsira cifundo pamaso pa mafumu a Perisiya, kuti atitsitsimutse kuimika nyumba ya Mulungu wathu, ndi kukonzanso muunda wace, ndi kutipatsa linga m'Yuda ndi m'Yerusalemu.

10 Ndipo tsopano, Mulungu wathu, tidzanenanji pambuyo pa ici? pakuti tasiya malamulo anu,

11 amene munalamulira mwa atumiki anu aneneri ndi kuti, Dzikolo mumukako likhale colowa canu ndilo dziko lodetsedwa mwa cidetso ca anthu a m'maikomo, mwa zonyansa zao zimene zinalidzaza, kuyambira nsonga yina kufikira nsonga inzace ndi ucisi wao.

12 Cifukwa cace tsono, musamapereka ana anu akazi kwa ana ao amuna, kapena kutengera ana anu amuna ana ao akazi, kapena kufuna mtendere wao ndi kukoma kwao nthwawi yonse, kuti mukhale olimba, ndi kudya zokoma za m'dziko, ndi kulisiyira ana anu colowa ca ku nthawi yonse.

13 Ndipo zitatigwera zonsezi cifukwa ca nchito zathu zoipa ndi kuparamula kwathu kwakukuru; popeza inu Mulungu wathu mwatilanga moticepsera mphulupulu zathu, ndi ku tipatsa cipulumutso cotere;

14 kodi tidzabwereza kuphwanya malamulo anu, ndi kukwatana nayo mitundu ya anthu ocita zonyansa izi? Simudzakwiya nafe kodi mpaka mwatitha, ndi kuti pasakhale otsala kapena akupulumuka?

15 Yehova Mulungu wa Israyeli, Inu ndinu wolungama, popeza tinatsala opulumuka monga lero lino; taonani, tiri pamaso panu m'kuparamula kwathu; pakuti palibe wakuima pamaso panu cifukwa ca ici.

10

1 Pakupemphera Ezara tsono, ndi kuulula ndi kulira misozi, ndi kudzigwetsa pansi pakhomo pa nyumba ya Mulungu, udamsonkhanira mwa Israyeli msonkhano waukuru ndithu wa amuna, ndi akazi, ndi ana; popeza anthu analira kulira, kwakukuru.

2 Pamenepo Sekaniya mwana wa Yehiyeli, mwana wina wa Elamu, anambwezera Ezara mau, nati, Talakwira Mulungu wathu, tadzitengera akazi acilendo a mitundu ya dzikoli; koma tsopano cimtsalira Israyeli ciyembekezo kunena za cinthu ici.

3 Ndipo tsono tipangane ndi Mulungu wathu kucotsa akazi onse, ndi obadwa mwa iwo, monga mwa uphungu wa mbuye wanga, ndi wa iwo akunjenjemera pa lamulo la Mulungu wathu; ndipo cicitike monga mwa cilamulo.

4 Nyamukani, mlandu ndi wanu; ndipo ife tiri nanu; limbikani, citani.

5 Nanyamuka Ezara, nalumbiritsa akulu a ansembe, ndi Alevi, ndi Aisrayeli onse, kuti adzacita monga mwa mau awa. Nalumbira iwo.

6 Pamenepo Ezara ananyamuka pakhomo pa nyumba ya. Mulungu, nalowa m'cipinda ca Yehohanana mwana wa Eliyasibu, ndipo atafikako sanadya mkate, sanamwa madzi; pakuti anacita maliro cifukwa ca kulakwa kwa iwo otengedwa ndende.

7 Nabukitsa iwo mau mwa Yuda ndi Yerusalemu kwa ana onse otengedwa ndende, kuti azisonkhana ku Yerusalemu;

8 ndi kuti ali yense wosafikako atapita masiku atatu, monga mwa uphungu wa akalonga ndi akuru, cuma cace conse cidzaonongeka konse, ndipo iye adzacotsedwa ku msonkhano wa iwo otengedwa ndende.

9 Ndipo anasonkhana ku Yerusalemu amuna onse a Yuda ndi Benjamini asanapite masiku atatu, ndiwo mwezi wacisanu ndi cinai, tsiku la makumi awiri a mwezi; nakhala pansi anthu onse m'khwalala pakhomo pa nyumba ya Mulungu, alikunjenjemera cifukwa ca mlandu uwu, ndi cifukwa ca mvulayi.

10 Pamenepo Ezara wansembe ananyamuka, nanena nao, Mwalakwa, mwadzitengera akazi acilendo, kuonjezera kuparamula kwa Israyeli.

11 Cifukwa cace tsono, ululani kwa Yehova Mulungu wa makolo anu, nimucite comkondweretsa; mudzilekanitse ndi mitundu ya anthu a m'dzikomo, ndi kwa akazi acilendo.

12 Ndipo unayankha msonkhano wonse, ndi kunena ndi mau akuru, Monga mwa mau anu tiyenera kucita.

13 Koma anthu ndiwo ambiri, ndi nyengo yino nja mvula, tiribenso mphamvu yakuima pabwalo, ndi nchitoyi sindiyo ya tsiku limodzi kapena awiri; pakuti tacurukitsa kulakwa kwathu pa cinthu ici.

14 Ayang'anire ici tsono akalonga athu a msonkhano wonse, ndi onse a m'midzi mwathu amene anadzitengera akazi acilendo abwere pa nthawi zoikika, ndi pamodzi nao akuru a mudzi wao uli wonse, ndi oweruza ace, mpaka udzaticokera mkwiyo waukali wa Mulungu wathu cifukwa ca mlandu uwu.

15 Yonatani mwana wa Asaheli ndi Yazeya mwana wa Tikiva okha anatsutsana naco, ndi Mesulamu ndi Sabetai Mlevi anawathandiza.

16 Pamenepo anthu otengedwa ndende anacita cotero. Ndi Ezara wansembe, ndi anthu akuru a nyumba za makolo, monga mwa nyumba za makolo ao, iwo onse ochulidwa maina ao anasankhidwa, nakhala pansi tsiku loyamba la mwezi wakhumi kufunsa za mlanduwu.

17 Natsiriza nao amuna onse adadzitengera akazi acilendo tsiku loyamba la mwezi woyamba.

18 Ndipo anapeza mwa ana a ansembe odzitengera akazi acilendo, ndiwo a ana a Yesuwa mwana wa Yozadaki, ndi abale ace Maseya, ndi Eliezere, ndi Yaribu, ndi Gedaliya.

19 Ndipo anaimika dzanja lao kuti adzacotsa akazi ao; ndipo popeza adaparamuladi, anapereka nsembe nkhosa yamphongo ya zoweta pa kuparamula kwao.

20 Ndi a ana a Imeri: Hanani ndi Zebadiya.

21 Ndi a ana a Harimu: Maseya, ndi Eliya, ndi Semaya, ndi Yehiyeli, ndi Uziya.

22 Ndi a ana a Pasuru: Elioenai, Maseya, Ismayeli, Netaneli, Yozabadi, ndi. Elasa.

23 Ndi a Alevi: Yozabadi, ndi Simei, ndi Kelaya (ndiye Kelita), Petahiya, Yuda, ndi Eliezere.

24 Ndi a oyimbira: Eliasibu; ndi a odikira: Salumu, ndi Telemu, ndi Uri.

25 Ndi Aisrayeli a ana a Parosi: Ramiya, ndi Iziya, ndi Matikiya, ndi Miyamini, ndi Eleazara, ndi Malikiya, ndi Benaya.

26 Ndi a ana a Elamu: Mataniya, Zekariya, ndi Yehieli, ndi Abidi, ndi Yeremoti, ndi Eliya.

27 Ndi a ana a Zatu: Elioenai, Eliasibi, Mataniya, ndi Yeremoti, ndi Zabadi, ndi Aziza.

28 Ndi a ana a Bebai: Yehohanana, Hananiya, Zabai, Atilai.

29 Ndi a ana a Bani: Mesulamu, Makuli, ndi Adaya, Yasubi, ndi Seali, Yeremoti.

30 Ndi a ana a Pahati: Moabu, Adina, ndi Kelali, Benaya, Maseya, Mataniya, Bezaleli, ndi Binui, ndi Manase.

31 Ndi a ana a Harimu: Eliezere, Isiya, Malikiya, Semaya, Simeoni,

32 Benjamini, Maluki, Semariya.

33 A ana a Hasumu: Matenai, Matata. Zabadi, Elifeleti, Yeremai, Manase, Simei.

34 A ana a Bani: Madai, Amiramu, ndi Ueli,

35 Benaya, Bedeya, Kelui,

36 Vaniya, Meremoti, Eliasibi,

37 Mataniya, Matenai, ndi Yasu,

38 ndi Bani, ndi Binui, Simei,

39 ndi Selemiya, ndi Natani, ndi Adaya,

40 Makinadebai, Sasai, Sarai,

41 Azareli, ndi Seleimiya, Semariya,

42 Salumu, Amariya, Yosefe.

43 A ana a Nebo: Yeieli, Matitiya, Zabadi, Zebina, Ido, ndi Yoeli, Banaya,

44 Awa onse adatenga akazi acilendo, ndi ena a iwowa anali ndi akazi amene adawabalira ana.