1

1 NDIPO atafa Yoswa, ana a Israyeli anafunsira kwa Yehova ndi kuti, Adzayamba ndani kutikwerera pa Akanani kuwathira nkhondo?

2 Ndipo Yehova anati, Akwere Yuda; taonani, ndapereka dzikoli m'dzanja lace.

3 Ndipo Yuda ananena ndi Simeoni mkuru wace, Kwera nane ku gawo langa kuti tiwathire nkhondo Akanani; ndipo inenso ndidzamuka nawe ku gawo lako. Namuka naye Simeoni.

4 Ndipo Yuda atakwera, Yehova anapereka Akanani ndi Aperizi m'dzanja lao, ndipo anakantha a iwowa anthu zikwi khumi.

5 Ndipo anapeza Adoni-bezeki m'Bezeki, namthira nkhondo nakantha Akanani ndi Aperizi.

6 Koma Adoni-bezeki anathawa; ndipo anampitikitsa, namgwira, namdula zala zazikuru za m'manja ndi za m'mapazi.

7 Pamenepo anati Adoni-bezeki, Mafumu makumi asanu ndi awiri odulidwa zala zazikuru za m'manja ndi m'mapazi anaola kakudya kao pansi pa gome panga; monga ndinacita ine, momwemo Mulungu wandibwezera. Ndipo anadza naye ku Yerusalemu, nafa iye komweko.

8 Ndipo ana a Yuda anacita nkhondo pa Yerusalemu, naulanda, naukantha ndi lupanga lakuthwa, natentha mudzi ndi moto.

9 Ndipo atatero ana a Yuda anatsika kuthirana nao nkhondo Akanani akukhala kumapiri, ndi kumwela ndi kucidikha.

10 Ndipo Yuda anamuka kwa Akanani akukhala m'Hebroni; koma kale dzina la Hebroni ndilo mudzi wa Ariba; ndipo anakantha Sesai, ndi Ahimani, ndi Talimai.

11 Pocoka pamenepo anamuka kwa nzika za ku Dibiri, koma kale dzina la Dibiri ndilo mudzi wa Seferi.

12 Ndipo Kalebe anati, iye amene akantha mudzi wa Seferi, naulanda, yemweyo ndidzampatsa Akisa mwana wanga wamkazi akhale mkazi wace.

13 Ndipo Otiniyeli, mwana wa Kenazi mng'ono wa Kalebi anaulanda, ndipo anampatsa Akisa mwana wace wamkazi akhale mkazi wace.

14 Ndipo kunali, m'mene anamdzera, anamkakamiza mwamuna wace kuti apemphe atate wace ampatse munda; natsika pa buru wace; ndipo Kalebe ananena naye, Ufunanji?

15 Ndipo anati kwa Iye, Mundipatse dalitso; popeza mwandipatsa dziko lakumwela, ndipatsenso zitsime za madzi. Pamenepo Kalebe anampatsa zitsime za kumtunda ndi zitsime za kunsi.

16 Ndipo ana a Mkeni mlamu wace wa Mose, anakwera kuturuka m'mudzi wa m'migwalangwa pamodzi ndi ana a Yuda, nalowa m'cipululu ca Yuda cokhala kumwela kwa Aradi; namuka iwo nakhala ndi anthuwo.

17 Ndipo Yuda anamuka ndi Simeoni mkuru wace, nakantha Akanani akukhala m'Zefati, nauononga konse. Koma dzina la mudziwo analicha Horima.

18 Yuda analandanso Gaza ndi malire ace, ndi Asikeloni ndi malire ace, ndi Ekroni ndi malire ace.

19 Ndipo Yehova anali ndi Yuda, iye nawaingitsa a kumapiri, osaingitsanzika za kucigwa, popeza zinali nao magareta acitsulo.

20 Ndipo anapatsa Kalebe Hebroni monga Mose adanena; iye nawaingitsa komweko ana amuna atatu a Anaki.

21 Koma ana a Benjamini sanaingitsa Ayebusi okhala m'Yerusalemu; koma Ayebusi anakhala m'Yerusalemu pamodzi ndi ana a Benjamini, mpaka lero lino.

22 Ndipo anakwera iwo a m'nyumba ya Yosefe naonso kumka ku Beteli; ndipo Yehova anakhala nao.

23 Ndipo iwo a m'nyumba ya Yosefe anatumiza ozonda ku Beteli. Koma kale dzina la mudziwo ndilo Luzi.

24 Ndipo alonda anaona munthu alikuturuka m'mudzi, nanena naye, Utionetsetu nolowera m'mudzi, ndipo tidzakucitira cifundo.

25 Nawaonetsa polowera m'mudzi iye, naukantha mudzi iwowa ndi lupanga lakuthwa; koma analola munthuyo ndi banja lace lonse amuke.

26 Ndipo munthuyo anamuka ku dziko la Ahiti, namanga mudzi, naucha dzina lace Luzi; ndilo dzina lace mpaka lero lino.

27 Koma Manase sanaingitsa a ku Betiseani ndi midzi yace kapena a Taanaki ndi midzi yace, kapena nzika za ku Dori ndi midzi yace, kapena nzika za ku Ibleamu ndi midzi yace, kapena nzika za ku Megido ndi midzi yace; koma Akanani anakhumba kukhala m'dziko muja.

28 Ndipo kunali, atakula mphamvu Israyeli, anasonkhetsa Akanani, osawaingitsa onse.

29 Ndipo Efraimu sanaingitsa Akanani okhala m'Gezeri; koma Akanani anakhala m'Gezeri pakati pao,

30 Zebuloni sanaingitsa nzika za ku Kitroni, kapena nzika za ku Nahaloli; koma Akanaru anakhala pakati pao, nawasonkhera.

31 Aseri sanaingitsa nzika za ku Ako, kapena nzika za ku Sidoni, kapena a Akalabu, kapena a Akisibu, kapena a Heliba, kapena a Afiki, kapena a Rehobo;

32 koma Aseri anakhala pakati pa Akanani nzika za kudziko; pakuti sanawaingitsa.

33 Nafitali sanaingitsa nzika za ku Beti-semesi, kapena nzika za ku Beri-anati; koma anakhala pakati pa Akanani, nzika za kudziko; koma nzika za ku Beti-semesi, ndi a ku Beti-anati zinawasonkhera.

34 Ndipo Aamori anakankha ana a Dani akhale kumapiri pakuti sanawalola atsikire kucigwa;

35 Aamori anakhumbanso kukhala ku phiri la Heresi, ku Ajaloni, ndi ku Saalibimu; koma dzanja la a m'nyumba ya Yosefe linawalaka, nakhala iwo akupereka msonkho.

36 Ndipo malire a Aamori anayambira pokwerera pa Akrabimu, pathanthwe, ndi pokwererapo.

2

1 Ndipo mthenga wa Yehova anakwera kucokera ku Giligala kumka ku Bokimu. Ndipo anati, Ndinakukweretsani kucokera ku Aigupto, ndi kulowetsa inu m'dziko limene ndinalumbirira makolo anu; ndipo ndinati, Sindidzathyola cipangano canga nanu ku nthawi yonse;

2 ndipo inu, musamacita pangano ndi nzika za m'dziko ili; muzigamula maguwa ao a nsembe. Koma simunamvera mau anga; mwacicita ici cifukwa ninji?

3 Cifukwa cacenso ndinati, Sindidzawapitikitsa kuwacotsa pamaso panu; koma adzakhala ngati minga m'nthiti zanu, ndi milungu yao idzakhalira inu msampha.

4 Ndipo kunali, pamene mthenga wa Yehova ananena mau awa kwa ana onse a Israyeli, anthuwo anakweza mau ao, nalira misozi.

5 Potero analicha dzina la malowo Bokimu: namphera Yehova nsembe pomwepo.

6 Pamene Yoswa atawalola anthu amuke, ana a Israyeli anamuka, yense ku colowa cace, dziko likhale lao lao.

7 Ndipo anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a Yoswa ndi masiku onse a akulu akulu otsala atafa Yoswa, amene adaona nchito yaikuru yonse ya Yehova anaicitira Israyeli.

8 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova anafa wa zaka zace zana ndi khumi.

9 Ndipo anamuika m'malire a colowa cace m'Timinatiheresi, ku mapiri a Efraimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.

10 Ndiponso mbadwo uwu wonse unasonkhanidwa kuikidwa kwa makolo ao; nuuka mbadwo wina pambuyo pao; wosadziwa Yehova kapena nchitoyi adaicitira Israyeli,

11 Ndipo ana a Israyeli anacita coipa pamaso pa Yehova, natumikira Abaala;

12 nasiya Yehova Mulungu wa makolo ao, amene adawaturutsa m'dziko la Aigupto, natsata milungu yina, milungu ya mitundu ya anthu okhala pozungulira pao, naigwadira; nautsa mkwiyo wa Yehova.

13 Ndipo anasiya Yehova, natumikira Baala ndi Asitaroti.

14 Pamenepo mkwiyo wa Yehova unayakira Israyeli, ndipo anawapereka m'manja a ofunkha kuti awafunkhe; nawagulitsa m'dzanja la adani ao akuwazungulira osakhozanso iwowo kuima pamaso pa adani ao.

15 Kuli konse anaturuka, dzanja la Yehova linawakhalira moipa, monga Yehova adanena, ndi monga Yehova adawalumbirira; nasautsika kwambiri iwowa.

16 Ndipo Yehova anautsa oweruza, amene anawapulumutsa m'dzanja la iwo akuwafunkha.

17 Koma sanamvera angakhale oweruza ao, pakuti anamuka kupembedza milungu yina, naigwadira; anapambuka msanga m'njira yoyendamo makolo ao, pomvera malamulo a Yehova; sanatero iwowa.

18 Ndipo pamene Yehova anawaukitsira oweruza, Yehova anakhala naye woweruzayo, nawapulumutsa m'dzanja la adani ao masiku onse a woweruzayo; pakuti Yehova anagwidwa cisoni pa kubuula kwao cifukwa ca iwo akuwapsinja ndi kuwatsendereza.

19 Koma kunali atafa woweruzayo anabwerera m'mbuyo, naposa makolo ao ndi kucita moipitsa, ndi kutsata milungu yina kuitumikira ndi kuigwadira, sanaleka kanthu ka macitidwe ao kapena ka njira yao yacheni.

20 Ndipo mkwiyo wa Yehova unayakira Israyeli; nati Iye, Popezamtundu uwu unalakwira cipangano canga cunene ndinalamulira makolo ao, osamvera mau ansa;

21 lnenso sindionjeza kuingitsa pamaso pao a mitundu yina imene Yoswa adaisiya pakufa iyeyu;

22 kuti ndiyese nayo Israyeli ngati adzasunga njira ya Yehova kuyendamo monga anaisunga makolo ao, kapena iai.

23 Motero Yehova analeka mitundu iyi osaiingitsa msanga, ndipo sadaipereka m'dzanja la yoswa.

3

1 Ndipo iyo ndiyo mitundu ya anthu anaisiyapo Yehova kuyesa nayo Israyeli, ndiwo onse amene sanadziwa nkhondo zonse za Kanani;

2 cifukwa cace ndico cokha cakuti adziwitse mibadwo ya ana a Israyeli ndi kuwaphunzitsa nkhondo, ngakhale iwo okha okha osaidziwa konse kale;

3 anasiya mafumu asanu a Afilisti ndi Akanani onse, ndi Asidoni, ndi Ahivi okhala m'phiri la Lebano, kuyambira phiri la Baalaherimoni mpaka polowera ku Hamati.

4 Amenewo anakhala coyesera Israyeli kuti Yehova adziwe ngati adzamvere malamulo ace, amene analamulira makolo ao mwa dzanja la Mose.

5 Ndipo ana a Israyeli anakhala pakati pa Akanani, Ahiti, ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi;

6 nakwatira ana akazi a iwowa, napereka ana ao akazi kwa ana amuna a iwowa natumikira milungu yao.

7 Ndipo ana a Israyeli anacita coipa pamaso pa Yehova, naiwala Yehova Mulungu wao, natumikira Abaala ndi zifanizo.

8 Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unayakira Israyeli ndipo anawagulitsa m'dzanja la KusaniRisataimu, mfumu ya Mesopotamiya; ndi ana a Israyeli anatumikira Kusani-Risataimu zaka zisanu ndi zitatu.

9 Ndipo pamene ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova, Yehova anaukitsira ana a Israyeli mpulumutsi amene anawapulumutsa, ndiye Otiniyeli mwana wa'Kenazi, mng'ono wace wa Kalebe.

10 Ndipo unamdzera mzimu wa Yehova, iye naweruza Israyeli, naturuka kunkhondo; napereka Yehova Kusani-Risataimu mfumu ya Mesapotamiya m'dzanja lace; ndi dzanja lace linamlaka Kusani-Risataimu.

11 Pamenepo dziko linapumula zaka makumi anai; ndi Otiniveli mwana wa Kenazi anafa.

12 Koma ana a Israyeli anaonjezanso kucita coipa pamaso pa Yehova; pamenepo Yehova analimbitsa Egiloni mfumu ya Moabu pa Israyeli, popeza anacita coipa pamaso pa Yehova.

13 Ndipo anadzisonkanitsira ana a Amoni ndi a Amaleki, namuka nakantha Israyeli, nalanda mudzi wa m'migwalangwa nakhalamo.

14 Ndipo ana a Israyeli anatumildra Egiloni mfumu ya Moabu zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu.

15 Koma pamene ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova, Yehova anawaukitsira mpulumutsi, Ehudi mwana wa Gera, Mbenjamini, munthu wamanzere, ndipo ana a Israyeli anatumiza mtulo m'dzanja lace Ikwa Egiloni mfumu ya Moabu.

16 Ndipo Ehudi anadzisulira lupanga lakuthwa konse konse utali wace mkono; nalimangirira pansi pa zobvala zace pa ncafu ya kulamanja.

17 Ndipo anapereka mtulo kwa Egiloni, mfumu ya Moabu; koma Egiloni ndiye munthu wonenepa ndithu.

18 Ndipo atatha kupereka mtulowo, anauza anthu onyamula mtulo acoke.

19 Koma iye mwini anabwerera pa mafano osema ali ku Giligala, nati, Ndiri nao mau acinsinsi kwa inu, mfumu. Nati iye, Khalani cete. Ndipo anaturuka onse akuimapo.

20 Ndipo Ehudi anamdzera alikukhala pa yekha m'cipinda cosanja copitidwa mphepo, Nati Ehudi, Ndiri nao mau a Mulungu akukuuzani. Nauka iye pa mpando wace.

21 Ndipo Ehudi anaturutsa dzanja lace lamanzere nagwira lupanga ku ncafu ya kulamanja nampyoza m'mimba mwace;

22 ndi cigumbu cace cinalowa kutsata mpeni wace; ndi mafuta anaphimba mpeniwo, pakuti sanasolola lupanga m'mimba mwace; nilituruka kumbuyo.

23 Pamenepo Ehudi anaturuka kukhonde namtsekera pamakomo pa cipinda cosanja nafungulira.

24 Ndipo ataturuka iye, anadza aka polo ace; napenya, ndipo taonani pamakomo pa cipinda cosanja mpofungulira; nati iwo, Angophimba mapazi m'cipinda cace cosanja copitidwa mphepo.

25 Ndipo analindirira mpaka anacita manyazi; koma taonani, sanatsegula pamakomo pa cipinda cosanja. Pamenepo anatenga mfungulo natsegula; ndipo taonani, mbuye wao wagwa pansi, wafa.

26 Ndipo Ehudi anapulumuka pakucedwa iwo, napitirira pa mafano osema, napulumuka kufikira Seira.

27 Ndipo kunali, pakufika iye anaomba lipenga ku mapiri a Efraimu; ndi ana a Israyeli anatsika naye kucokera kumapiri, nawatsogolera iye.

28 Ndipo ananena nao, Nditsateni ine, pakuti Yehova wapereka adani anu Amoabu m'manja mwanu. Ndipo anatsika ndi kumtsata, natsekereza Amoabu madooko a Yordano, osalola mmodzi aoloke.

29 Ndipo anakantha Amoabu nyengo ija anthu zikwi khumi, onsewa anthu amoyo, ndi ngwazi; ndipo sanapulumuka ndi mmodzi yense.

30 Motero anagonjetsa Moabu tsiku lija pansi pa dzanja la Israyeli. Ndipo dziko linapumulazaka makumi asanu ndi atatu.

31 Atapita iye kunali Samagara, mwana wa Anati amene anakantha Afilisti mazana asanu ndi limodzi ndi mtoso wa ng'ombe; nayenso anapulumutsa Israyeli.

4

1 Ndipo ana a Israyeli anaonjeza kucita coipa pamaso pa Yehova, atafa Ehudi.

2 Ndipo Yehova anawagulitsa m'dzanja la Yabini mfumu ya Kanani, wocita ufumu ku Hazori; kazembe wace wa nkhondo ndiye Sisera, wokhala ku Haroseti wa amitundu.

3 Ndipo ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova; pakuti anali nao magareta acitsulo mazana asanu ndi anai; napsinja ana a Israyeli kolimba zaka makumi awiri.

4 Ndipo Debora, mneneri wamkazi, ndiye mkazi wace wa Lapidoti, anaweruza Israyeli nyengo ija,

5 Ndipo anakhala patsinde pa mgwalangwa wa Debora pakati pa Rama ndi Beteli ku mapiri a Efraimu; ndi ana a Israyeli anakwera kwa iye awaweruze.

6 Ndipo anatuma, naitana Baraki mwana wa Abinoamu, acoke m'Kedesi-Nafitali; nanena naye, Kodi Yehova Mulungu wa Israyeli sanalamulira ndi kuti, Muka, nuluniike ku phiri la Tabori, nuwatenge, apite nawe anthu zikwi khumi a ana a Nafitali ndi ana a Zebuloni?

7 Ndipo ndidzamkoka Sisera, kazembe wa nkhondo ya Yabini, akudzere ku mtsinje wa Kisoni, ndi magareta ace, ndi aunyinji ace; ndipo ndidzampereka m'dzanja lako.

8 Ndipo Baraki anati kwa iye, Ukamuka nane, ndidzamuka; ukapanda kumuka nane, sindimuka.

9 Nati iye, Kumuka ndidzamuka nawe, koma ulendo umukawo, sudzacita nao ulemu; pakuti: Yehova adzagulitsa Sisera m'dzanja la mkazi, Motero Debora anauka namuka ndi Baraki ku Kedesi.

10 Ndipo Baraki anaitana Zebuloni ndi Nafitali asonkhane ku Kedesi; iye nakwera ndi anthu zikwi khumi akumtsata; Deboranso anakwera kumka naye.

11 Ndipo Heberi Mkeni anadzisiyanitsa ndi Akeni, ndi ana a Hobabu mlamu wace wa Mose, namanga mahema ace mpaka thundu wa m'Zaananimu, ndiwo wa ku Kedesi.

12 Ndipo anauza Sisera kuti Baraki mwana wa Abinoamu wakwera ku phiri la Tabori.

13 Pamenepo Sisera anasonkhanitsa magareta ace onse ndiwo magareta mazana asanu ndi anai acitsulo, ndi anthu onse okhala naye, kuyambira Haroseti wa amitundu mpaka mtsinje wa Kisoni.

14 Ndipo Debora anati kwa Baraki, Nyamuka; pakuti ili ndi tsikuli Yehova wapereka Sisera m'dzanja lako; sanaturuka kodi Yehova pamaso pako? Potero Baraki anatsika ku phiri la Tabori ndi amuna zikwi khumi akumtsata.

15 Ndipo Ambuye anaononga Sisera, ndi magareta onse ndi gulu lankhondo lonse, adi lupanga lakuthwa pamaso pa Baraki; koma Sisera anatsika pagareta nathawa coyenda pansi.

16 Koma Baraki anatsata magareta ndi gululo mpaka Haroseti wa amitundu; ndi gulu lonse lankhondo la Sisera linagwa ndi lupanga lakuthwa, sanatsala munthu ndi mmodzi yense.

17 Koma Sisera anathawira coyenda pansi ku hema wa Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni; pakuti panali mtendere pakati pa Yabini mfumu ya Hazori, ndi nyumba ya Heberi Mkeni.

18 Ndipo Yaeli anaturuka kukomana ndi Sisera, nanena naye, Pambuka, mbuye wanga, pambukira kwa ine kuno; usaope. Ndipo anapambukira kwa iye kulowa m'hema, nampfunda ndi cimbwi.

19 Pamenepo ananena naye, Ndipatsetu madzi pang'ono ndimwe; popeza ndine waludzu. Ndipo anatsegula thumba la mkaka, nampatsa amwe, nampfunda.

20 Ndipo Sisera ananena naye, Taima pakhomo pa hema, ndipo kudzali, akadza munthu, akakufunsa akati, Pali munthu pano kodi? Uziti, Palibe.

21 Pamenepo Yaeli mkazi wa Heberi anatenga ciciri ca hema, natenga nyundo m'dzanja lace namdzera monyang'ama, nakhomera ciciri cilowe m'litsipa mwace; nicinapyoza kulowa m'nthaka; popeza anali m'tulo tofa nato ndi kulema; nafa.

22 Ndipo taonani, pomlondola Sisera Barakiyo, Yaeli anaturuka kukomana naye, Dati kwa iye, Idza kuno, ndidzakuonetsa munthu umfunayo, Potero anamdzera, ndipo taonani, Sisera wagwa, wafa, ndi ciciri m'litsipa mwace.

23 Momwemo Mulungu anagonjetsa tsiku lija Yabini mfumu ya Kanani pamaso pa ana a Israyeli.

24 Ndipo dzanja la ana a Israyeli linamkabe ndi kulimbika pa Yabini mfumu ya Kanani mpaka adamuononga Yabini mfumu ya Kanani.

5

1 Ndipo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba tsiku lomwelo ndi kuti,

2 Lemekezani Yehova Pakuti atsogoleri m'Israyeli anatsogolera, Pakuti anthu anadzipereka mwaufulu.

3 Imvani mafumu inu; cherani makutu, akalonga inu; Ndidzayimbira ine Yehova, inetu; Ndidzamuyimbira nyimbo, Yehova, Mulungu wa Israyeli,

4 Yehova, muja mudaturuka m'Seiri, Muja mudayenda kucokera ku thengo la Edomu, Dziko linanjenjemera, thambo lomwe linakha, Inde mitambo inakha madzi.

5 Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova, Sinai ili pamaso pa Yehova, Mulungu wa Israyeli.

6 Masiku a Samagara, mwana wa Anati, Masiku a Yaeli maulendo adalekeka Ndi apanjira anayenda mopazapaza,

7 Miraga idalekeka m'Israyeli, idalekeka. Mpaka ndinauka ine Debora, Ndinauka ine amai wa Israyeli.

8 Anasankha milungu yatsopano, Pamenepo nkhondo inaoneka kuzipata. Ngati cikopa kapena nthungo zidaoneka Mwa zikwi makumi anai a Israyeli?

9 Mtima wanga ubvomerezana nao olamulira a m'Israyeli, Amene anadzipereka mwaufulu mwaanthu. Lemekezani Yehova.

10 Inu akuyenda okwera pa aburu oyera, Inu akukhala poweruzira, Ndi inu akuyenda m'njira, fotokozerani.

11 Posamveka phokoso la amauta potunga madzi, Pomwepo adzafotokozera zolungama anazicita Yehova, Zolungama anazicita m'miraga yace, m'lsrayeli. Pamenepo anthu a Yehova anatsikira kuzipata.

12 Galamuka, Debora, galamuka, Galamuka, galamuka, unene nyimbo; Uka, Baraki, manga nsinga ndende zako, mwana wa Abinoamu, iwe.

13 Pamenepo omveka otsala anatsika ndi anthu; Yehova ananditsikira pakati pa acamuna.

14 Anafika Aefraimu amene adika mizu m'Amaleki; Benjamini anakutsata iwe pakati pa anthu ako. Ku Makiri kudacokera olamulira, Ndi ku Zebuloni iwo akutenga ndodo ya mtsogoleri.

15 Akalonga a Isakara anali ndi Debora; Monga Isakara momwemo Baraki, Anawatuma m'cigwa namka coyenda pansi. Pa mitsinje ya Rubeni panali zotsimikiza mtima zazikuru.

16 Wakhaliranji pakati pa makola, Kumvera kulira kwa zoweta? Ku timitsinje ta Rubeni kunali zotsimikiza mtima zazikuru.

17 Gileadi anakhala tsidya lija la Yordano; Ndi Dani, akhaliranji mzombo? Aseri anakhala pansi m'mphepete mwa nyanja, Nakhalitsa pa nyondo yace ya nyanja.

18 Zebuloni ndiwo anthu anataya moyo wao mpaka imfa, Nafitali yemwe poponyana pamisanje.

19 Anadza mafumu, nathira nkhondo Pamen'epo anathira nkhondo mafumu a Kanani. M'Taanaki, ku madzi a Megido; Osatengako phindu la ndarama.

20 Nyenyezi zinathira nkhondo yocokera kumwamba, M'mipita mwao zinathirana ndi Sisera.

21 Mtsinje wa Kisoni unawakokolola, Mtsinje uja wakale, mtsinje wa Kisoni. Yenda mwamphamvu, moyo wangawe.

22 Pamenepo ziboda za akavalo zinaguguda, Ndi kutumphatumpha, kurumphatumpha kwa anthu ace eni mphamvu,

23 Mutemberere Merozi, ati mthenga wa Yehova, Mutemberere citemberere nzika zace; Pakuti sanadzathandiza Yehova, Kumthandiza Yehova pa acamuna.

24 Wodalitsika, woposa akazi, akhale Yaeli Mkazi wa Heberi Mkeni. Akhale wodalitsika woposa akazi a m'hema.

25 Mwamunayo anapempha madzi, anampatsa mkaka, Anamtengera mafuta a mkaka m'cotengera ca mfulu.

26 Dzanja lace analitambasulira kuciciri, Ndi dzanja lace lamanja ku nyundo ya anchito, Nakhomera Sisera, nakantha mutu wace, Inde, anaphwanya napyoza m'litsipa mwace.

27 Pa mapazi ace anabzong'onyoka, anagwa, anagona; Pa mapazi ace anabzong'onyoka, anagwa; Pobzong'onyokapo, pamenepo wagwa wafa.

28 Anapenyerera ali pazenera, napfuula Mace wa Sisera, pa made ace, Acedweranji gareta wace? Zizengerezeranji njinga za magareta ace?

29 Akazi anzace omveka anzeru anamyankha; Koma anadziyankhira yekha mau,

30 Kodi sanapeza, sanagawa zofunkha? Namwali, anamwali awiri kwa munthu ali yense. Cofunkha ca nsaru za mawanga mawanga kwa Sisera; Cofunkha ca nsaru za mawanga mawanga, za maluwa, Nsaru za mawanga mawanga, za maluwa konse konse, kwa cofunkha ca khosi lace.

31 Adani anu onse, Yehova, atayike momwemo. Koma iwo akukonda Inu akhale ngati dzuwa loturuka mu mphamvu yace. Ndipo dziko linapumula zaka makumi anai.

6

1 Koma ana a Israyeli anacita coipa pamaso pa Yehova; ndipo Yehova anawapereka m'dzanja la Midyani zaka zisanu ndi ziwiri.

2 Pamene dzanja la Midyani linalaka Israyeli, ana a Israyeli anadzikonzera ming'ang'ala ya m'mapiri, ndi mapanga, ndi malinga cifukwa ca Midyani.

3 Ndipo kunali, akabzala Israyeli, amakwera Amidyani, ndi Amaleki, ndi ana a kum'mawa, inde amawakwerera;

4 nawamangira misasa, namaononga zipatso za m'dziko mpaka ufika ku Gaza, osawasiyira cocirira njala m'Israyeli, ngakhale nkhosa, kapena ng'ombe, kapena buru.

5 Pakuti anakwera nazo zoweta zao ndi mahema ao, analowa ngati dzombe kucuruka kwao; iwowa ndi ngamila zao zomwe nzosawerengeka; ndipo analowa m'dziko kuliononga.

6 Ndipo Israyeli anafoka kwambiri cifukwa ca Midyani; ndipo ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova.

7 Ndipo kunali, pamene ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova cifukwa ca Midyani,

8 Yehova anatuma munthu mneneri kwa ana a Israyeli, nanena nao, Atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Ine ndinakukwezani kucokera m'Aigupto, ndi kukuturutsani m'nyumba ya ukapolo;

9 ndipo ndinakulanditsani m'dzanja la Aaigupto, ndi m'dzanja la onse akupsinja inu, ndi kuwaingitsa pamaso panu, ndi kukupatsani dziko lao;

10 ndipo ndinati kwa inu, Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musamaopa milungu ya Aamori amene mukhala m'dziko lao; koma simunamvera mau anga.

11 Pamenepo anadza mthenga wa Yehova, nakhala patsinde pa thundu wokhala m'Ofira, wa Yoasi M-abieziri; ndi mwana wace Gideoni analikuomba tirigu m'mopondera mphesa, awabisire Amidyani.

12 Ndipo mthenga wa Yehova anamuonekera, nati kwa iye, Yehova ali nawe, ngwazi iwe, wamphamvu iwe.

13 Ndipo Gideoni ananena naye, Mbuye wanga, ngati Yehova ali nafe catigwera ife bwanji conseci? ndipo ziti kuti zodabwiza zace zonse zimene makolo athu anatiwerengera, ndi kuti, Sanatikweza kodi Yehova kucokera m'Aigupto? Koma tsopano Yehova watitaya natipereka m'dzanja la Midyani.

14 Pamenepo Yehova anamtembenukira, nati, Muka nayo mphamvu yako iyi, nupulumutse Israyeli m'dzanja la Midyani, Sindinakutuma ndi Ine kodi?

15 Ndipo anati kwa iye, Ha! Mbuye, ndidzapulumutsa Israyeli ndi ciani? Taonani, banja langa liri loluluka m'Manase, ndipo ine ndine wamng'ono m'nyumba ya atate wanga.

16 Ndipo Yehova ananena naye, Popeza Ine ndidzakhala nawe udzakantha Amidyani ngati munthu mmodzi.

17 Ndipo anati kwa iye, Ngati mundikomera mtima mundionetse cizindikilo tsopano cakuti ndi Inu wakunena nane.

18 Musacoke pano, ndikupemphani, mpaka ndikudzerani ndi kuturutsa copereka canga ndi kuciika pamaso panu. Ndipo anati, Ndidzalinda mpaka ubwera.

19 Ndipo Gideoni analowa, nakonza kambuzi ndi mikate yopanda cotupitsa ya muyeso wa ufa; nyamayi anaiika m'licero, ndi msuzi anauthira mumbale, naturuka nazo kwa iye ali patsinde pa thundu, nazipereka.

20 Koma mthenga wa Mulungu ananena naye, Tenga nyamayi ndi mikate yopanda cotupitsa ndi kuziika pathanthwe pano ndi kutsanula msuzi. Ndipo anatero.

21 Pamenepo mthenga wa Yehova anatambasula nsonga ya ndodo inali m'dzanja lace, nakhudza nyamayi ndi mikate yopanda cotupitsa; ndipo unaturuka moto m'thanthwe nunyeketsa nyama ndi mikate yopanda cotupitsa; ndi mthenga wa Yehova anakanganuka pamaso pace.

22 Pamenepo Gideoni anaona kuti ndiye mthenga wa Yehova, nati Gideoni, Tsoka ine, Yehova Mulungu! popeza ndaona mthenga wa Yehova maso ndi maso.

23 Ndipo Yehova anati kwa iye, Mtendere ukhale ndi iwe, usaope, sudzafa.

24 Pamenepo Gideoni anammangira Yehova guwa la nsembe pomwepo; nalicha Yehova-ndiyemtendere; likali m'Ofira wa Abieziri ndi pano pomwe.

25 Ndipo kunali, usiku womwe uja Yehova ananena naye, Tenga ng'ombe ya atate wako, ndiyo ng'ombe yaciwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri, nugamule guwa la nsembe la Baala ndilo la atate wako, nulikhe cifanizo ciri pomwepo;

26 numangire Yehova Mulungu wako guwa la nsembe pamwamba pa lingali, monga kuyenera; nutenge ng'ombe yaciwiriyo, nufukize nsembe yopsereza; nkhuni zace uyese cifanizo walikhaco.

27 Pamenepo Gideoni anatenga amuna khumi mwa anyamata ace, nacita monga Yehova adanena naye; ndipo kunali, popeza anaopa a ku nyumba ya atate wace, ndi amuna a ku mudziwo, sanacicita msana, koma usiku.

28 Ndipo pakuuka mamawa amuna a ku mudziwo, taonani, guwa la nsembe la Baala litagamuka, ndi cifanizo cinali pomwepo citalikhidwa ndi ng'ombe yaciwiri yoperekedwa pa guwa la nsembe adalimanga.

29 Nanenana wina ndi mnzace, Wacita ici ndani? Ndipo atafunafuna nafunsafunsa, anati, Gideoni, mwana wa Yoasi wacita ici.

30 Pamenepo amuna a ku mudziwo anati kwa Yoasi, Umturutse mwana wako kuti afe; pakuti anagamula guwa la nsembe la Baala, pakutinso analikha cifanizo cinali pomwepo.

31 Koma Yoasi anati kwa onse akumuimirira, Kodi inu mumnenera Baala mlandu? Kapena kodi mudzampulumutsa iye? iye amene amnenera mlandu aphedwe kukali m'mawa; akakhala mulungu adzinenere yekha mlandu, popeza wina wamgamulira guwa lace la nsembe.

32 Cifukwa cace anamucha tsiku lija Yerubaala, ndi kuti, Amnenece mlandu Baala popeza anamgamulira guwa lace la nsembe.

33 Pamenepo Amidyani onse ndi Aamaleki ndi ana a kum'mawa anasonkhana pamodzi naoloka, namanga misasa m'cigwa ca Yezreeli.

34 Koma mzimu wa Yehova unabvana Gideoni; naomba lipenga iye, ndi a banja la Abieziri analalikidwa kumtsata iye.

35 Ndipo anatuma mithenga kwa Manase konse; ndi iwonso analalikidwa kumtsata iye; natuma mithenga kwa Aseri, ndi kwa Zebuloni, ndi kwa Nafitali; iwo nadzakomana nao.

36 Ndipo Gideoni anati kwa Mulungu, Mukadzapulumutsa Israyeli ndi dzanjalanga monga mwanena,

37 taonani, ndidzaika cikopa ca ubweya popunthira tirigu; pakakhala mame pacikopa pokha, ndi panthaka ponse pouma, pamenepo ndidzadziwa kuti mudzapulumutsa Israyeli ndi dzanja langa monga mwanena.

38 Ndipo kunatero; pakuti anauka mamawa, nafinya cikopaco, nakamula mame a pacikopa, madzi ace odzala mbale.

39 Ndipo Gideoni ananena ndi Mulungu, Mkwiyo wanu usandiyakire, ndinene kamodzi kokha: ndikuyeseni kamodzi kokha ndi cikopa; paume pacikopa pokha, ndi panthaka ponse pakhale mame.

40 Ndipo Mulungu anatero usiku uja; pakuti panauma pacikopa pokha, ndi panthaka ponse panali mame.

7

1 Pamenepo Yerubaala, ndiye Gideoni, ndi anthu onse okhala naye anauka mamawa, namanga misasa pa citsime ca Harodi, ndi misasa ya Midyani inali kumpoto kwao, pa phiri la More m'cigwa.

2 Ndipo Yehova anati kwa Gideoni. Anthu ali ndi iwe andicurukira kuti ndipereke Midyani m'dzanja lao; angadzitame Israyeli pa Ine, ndi kuti, Dzanja la ine mwini landipulumutsa.

3 Ndipo tsopano, kalalike m'makutu a anthu, ndi kuti, Ali yense wocita mantha, nanjenjemera, abwerere nacoke pa phiri la Gileadi. Ndipo anabwererako anthu zikwi makumi awiri mphambu ziwiri, natsalako zikwi khumi.

4 Ndipo Yehova ananena ndi Gideoni, Anthu akali ocuruka; tsikira nao kumadzi, ndipo ndidzakuyesera iwo komweko; ndipo kudzali kuti iye amene ndimnena kwa iwe, Uyo azimuka nawe, yemweyo azimuka nawe; koma ali yense ndimnena kwa iwe, Uyo asamuke nawe, yemweyo asamuke.

5 Ndipo anatsikira nao anthu kumadzi; ndipo Yehova anati kwa Gideoni, Ali yense akapiza madzi pa lilime lace, monga akhatira garu, ameneyo amuike pa yekha; momwemo ali yense agwada pakumwa.

6 Ndi kuwerenga kwa iwo akukhatira, ndi kuika dzanja lao kukamwa kwao, ndiko mazana atatu; koma ena onse anagwada pakumwa madzi.

7 Ndipo Yehova anati kwa Gideoni, Ndi anthu mazana atatu akukhatira ndidzakupulumutsani, ndi kupereka Amidyani m'dzanja lako; koma amuke anthu awa onse, yense kumalo kwace.

8 Pamenepo anthu anatenga kamba m'dzanja lao, ndi malipenga ao; ndipo anauza amuna onse a Israyeli amuke, yense kuhema kwace; koma anaimika amuna mazana atatuwo; ndipo misasa ya Midyani inali kunsi kwace m'cigwa.

9 Ndipo kunali usiku womwewo, kuti Yehova ananena naye, Tauka, tatsikira kumisasa; pakuti ndaipereka m'dzanja lako.

10 Koma ngati uopa kutsika, utsike naye Pura mnyamata wako kumisasa;

11 nudzamva zonena iwo; utatero manja ako adzalimbikitsidwa kutsikira kumisasa. Pamenepo anatsikira ndi Pura mnyamata wace ku cilekezero ca anthu azidaa m'misasa.

12 Ndipo Amidyani ndi Aamaleki ndi ana onse a kum'mawa ali gonere m'cigwa, kucuruka kwao ngati dzombe; ndi ngamila zao zosawerengeka, kucuruka kwao ngati mcenga wa m'mphepete mwa nyanja.

13 Ndipo pakufikako Gideoni, taonani, panali munthu analikufotokozera mnzace loto, nati, Taona, kulota ndinalota, ndipo tapenya, mtanda wa mkate wabarele unakunkhulira-kunkhulira m'misasa ya Midyani, nufika kuhema, numgunda nagwa, numpidigula kuti hema anakhala cigwere.

14 Ndipo mnzace anayankha nati, Ici si cina konse koma lupanga la Gideoni mwana wa Yoasi, munthu wa Israyeli; Mulungu wapereka Midyani ndi a m'misasa onse m'dzanja lace.

15 Ndipo kunali, pakumva Gideoni kufotokozera kwa lotolo ndi tanthauzo lace, anadziwerama; nabwera ku misasa ya Israyeli nati, Taukani, pakuti Yehova wapereka a m'misasa a Midyani m'dzanja lanu.

16 Ndipo anagawa amuna mazana atatu akhale magulu atatu, napatsa malipenga m'manja a iwo onse, ndi mbiya zopanda kanthu, ndi miuni m'kati mwa mbiyazo,

17 Ndipo ananena nao, Mundipenyerere ine, ndi kucita momwemo; ndipo taonani, pakufika ine pa cilekezero ca misasa, kudzali, monga ndicita ine, momwemo muzicita inu.

18 Pamene ndiomba lipenga, ine ndi onse okhala nane, inunso muziomba lipenga pozungulira ponse pa misasa, ndi kunena kuti, Yehova ndi Gideoni.

19 Motero Gideoni ndi amuna zana anali naye anafikira ku cilekezero ca misasa poyambira ulonda wa pakati, atasintha alonda tsopano apa; ndipo anaomba malipenga, naphwanya mbiya zokhala m'manja mwao.

20 Ndi magulu atatuwo anaomba malipenga, naswa mbiyazo, nagwira miuni ndi dzanja lao lamanzere, ndi malipenga m'dzanja lao lamanja kuwaomba; ndipo anapfuula, Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.

21 Ndipo anaima yense m'mbuto mwace pozungulira misasa; pamenepo anathamanga a m'misasa onse, napfuula, nathawa.

22 Ndipo mazana atatuwa anaomba malipenga, ndipo Yehova anakanthanitsa yense mnzace ndi lupanga m'misasa monse; ndi a m'misasa anathawa mpaka ku Betesita ku Zerera, mpaka ku malire a Abelemehola pa Tabati.

23 Pamenepo anthu a Israyeli analalikidwa kucokera ku Nafitali, ndi ku Aseri, ndi ku Manase yense, nalondola Amidyani.

24 Gideoni anatumanso mithenga ku mapiri onse a Efraimu ndi kuti, Tsikani, kukomana ndi Amidyani ndi kutsekereza madooko asanafike iwowa, mpaka ku Beti-bara ndi Yordano. Potero amuna onse a Efraimu anasonkhana pamodzi natsekereza madooko mpaka ku Betibara, ndi Yordano.

25 Ndipo anagwira akalonga awiri a Midyani, Orebi ndi Zeebi; namupha Orebi ku thanthwe la Orebi; ndi Zeebi anamupha ku coponderamo mphesa ca Zeebi, nalondola Amidyani; ndipo anadza nayo mitu ya Orebi ndi Zeebi kwa Gideoni tsidya lija la Yordano.

8

1 Ndipo amuna a Efraimu anati kwa iye, Ici waticitira nciani, osatiitana popita iwe kulimbana ndi Amidyani? natsutsana naye kolimba.

2 Koma ananena nao, Ndacitanji tsopano monga inu? Kodi kukunkha mphesa kwa Efraimu sikuposa kuchera mphesa kwa Abiezeri?

3 Mulungu anapereka m'dzanja lanu akalonga a Midyani, Orebi ndi Zeebi, ndipo ndinakhoza kucitanji monga inu? Pamenepo mkwiyo wao unamlezera, atanena mau awa.

4 Ndipo Gideoni anafika ku Yordano, naoloka, iye ndi amuna mazana atatu anali naye, ali otopa koma ali cilondolere.

5 Ndipo ananena kwa amuna a ku Sukoti, Mupatsetu anthu awa akunditsata mitanda yamkate; pakuti atopa, ndipo ndirikulondola Zeba ndi Tsalimuna mafumu a Midyani.

6 Koma akalonga a ku Sukoti anati, Kodi manja a Zeba ndi Tsalimuna ali m'dzanja lako tsopano apa, kuti ife tiwaninkhe ankhondo ako mkate?

7 Ndipo Gideoni anati, Cifukwa cace, Yehova akapereka Zeba ndi Tsalimuna m'dzanja langa, ndidzapuntha nyama yanu ndi minga ya m'cipululu ndi mitungwi.

8 Ndipo anacokapo kukwera ku Penueli, nanena nao momwemo; ndipo amuna a ku Penueli anamyankha monga adamyankha amuna a ku Sukoti.

9 Ndipo ananenanso kwa amuna a ku Penueli ndi kuti, Ndikabwerera ndi mtendere ndidzagumula nsanja iyi.

10 Zeba ndi Tsalimuna ndipo anali m'Karikori, ndi a m'misasa ao pamodzi nao, amuna monga zikwi khumi ndi zisanu; ndiwo otsala onse a khamu lonse la ana a kum'mawa; popeza atagwa amuna zikwi zana limodzi ndi makumi awiri akusolola lupanga.

11 Ndipo Gideoni anakwerera njira ya iwo okhala m'mahema kum'mawa kwa Noba, ndi Yogibea, nakantha khamulo popeza khamulo linakhala lokhazikika mtima.

12 Ndipo Zeba ndi Tsalimuna anathawa; koma anawatsata, nagwira mafumu awiri a Midyani Zeba ndi Tsalimuna, nanjenjemeretsa khamu lonse.

13 Pamenepo Gideoni mwana wa Yoasi anabwerera kunkhondo pokwerera pa Heresi.

14 Ndipo anagwira mnyamata wa anthu a ku Sukoti, nafunsira; ndipo anamsimbira akalonga a ku Sukoti, ndi akulu ace amuna makumi asanu ndi awiri kudza asanu ndi awiri.

15 Ndipo anafika kwa amuna a ku Sukoti, nati, Tapenyani Zeba ndi Tsalimuna amene munanditonza nao ndi kuti, Kodi manja a Zeba ndi Tsalimuna akhala m'dzanja lako, kuti tiwaninkhe mkate amuna ako akulema?

16 Ndipo anagwira akulu, a m'mudzi ndi minga ya kucipululu ndi mitungwi, nawalanga nazo amuna a ku Sukoti.

17 Ndipo anagamula nsanja ya Penueli, napha amuna a kumudzi.

18 Pamenepo anati kwa Zeba ndi Tsalimuna, Amunawo munawapha ku Tabori anali otani? Iwo nayankha, Monga iwe momwemo iwowa; yense wakunga mwana wa mfumu.

19 Ndipo anati, Ndiwo abale anga, ana a mai wanga. Pali Yehova mukadawasunga amoyo, sindikadakuphani.

20 Nati kwa Yeteri mwana wace woyamba, Tauka, nuwaphe. Koma mnyamatayo sanasolola lupanga lace; pakuti anaopa, pokhala anali mnyamata.

21 Pamenepo Zeba ndi Tsalimuna anati, Tauka iwe mwini nutigwere; pakuti monga munthu momwemo mphamvu yace. Ndipo Gideoni anauka nawapha Zeba ndi Tsalimuna, nalanda mphande zinali kukhosi kwa ngamila zao.

22 Pamenepo anthu a Israyeli anati kwa Gideoni, Mutilamulire ndi inu, ndi mwana wanu, ndi mdzukulu wanu, pakuti mwatipulumutsa m'dzanja la Amidyani.

23 Koma Gideoni ananena nao. Sindidzalamulira inu, ngakhale mwana wanga sadzalamulira inu; Yehova adzalamulira inu.

24 Gideoni anatinso kwa iwo, Mundilole ndipemphe kanthu kamodzi kwa inu, mundipatse ali yense mapelele mwa zofunkha zanu; pakuti anali nao mapelele agolidi, pokhala anali Aismayeli.

25 Ndipo anayankha, Kupereka tiwapereka; nayalapo cobvala, naponyamo yense mapelele a mwa zofunkha zao.

26 Ndipo kulemera kwace kwa mapelele agolidi adawapempha ndiko masekeli cikwi cimodzi ndi mazana asanu ndi awiri; osawerenga mphande, ndi zitunga ndi zobvala zacibakuwa za pa mafumu a ku Midyani, osawerenganso maunyolo okhala pa makosi a ngamila zao.

27 Ndipo Gideoni anawapanga fano, naliika m'mudzi mwace, ndiwo Ofira; ndi Israyeli yense analitsata kuligwadira pomwepo; ndipo linakhala kwa Gideoni ndi nyumba yace ngati msampha.

28 Motero anagonjetsa Amidyani pamaso pa ana a Israyeli, osaweramutsanso mitu yao iwowa. Ndipo dziko lidapumula zaka makumi anai m'masiku a Gideoni.

29 Ndipo Yerubaala, mwana wa Yoasi anamuka, nakhala, m'nyumba ya iye yekha.

30 Nakhala nao ana amuna makumi asanu ndi awiri Gideoni, anawabala ndi iye; popeza anali nao akazi ambiri.

31 Ndipo mkazi wace wamng'ono wokhala m'Sekemu, iyenso anambalira mwana wamwamuna; namucha dzina lace Abimeleki.

32 Ndipo Gideoni mwana wa Yoasi anafa atakalamba bwino, naikidwa m'manda a Yoasi atate wace, m'Ofira wa Aabiezeri.

33 Ndipo kunali, atafa Gideoni, ana a Israyeli anabwereranso nagwadira Abaala, nayesa Baala-beriti mulungu wao.

34 Ndi ana a Israyeli sanakumbukila Yehova Mulungu wao, amene anawapulumutsa m'dzanja la adani ao onse pozungulira ponse;

35 osacitira cifundo nyumba ya Yerubaala, ndiye Gideoni, monga mwa zokoma zonse iye anacitira Israyeli.

9

1 Koma Abimeleki mwana wa Yerubaala anamuka ku Sekemu kwa abale a amai wace, nanena nao, ndi kwa banja lonse la nyumba ya atate wa amai wace, ndi kuti,

2 Nenanitu m'makutu mwa eni ace onse a ku Sekemu, Cokomera inu nciti, akulamulireni ana amuna onse a Yerubaala ndiwo amuna makumi asanu ndi awiri, kapena akulamulireni mwamuna mmodzi? mukumbukilenso kuti ine ndine wa pfuko lanu ndi nyama yanu.

3 Pamenepo abale a amace anamnenera mau awa onse m'makutu a eni ace onse a Sekemu; ndi mitima yao inalunjika kutsata Abimeleki; pakuti anati, Ndiye mbale wathu.

4 Ndipo anampatsa ndalama makumi asanu ndi awiri za m'nyumba ya Baala-beriti; ndipo Abimeleki analembera nazo anthu opanda pace ndi opepuka amene anamtsata.

5 Ndipo anamuka ku nyumba ya atate wace ku Ofira, nawapha abale ace ana a Yerubaala, ndiwo amuna makumi asanu ndi awiri, pa thanthwe limodzi; koma Yotamu mwana wamng'ono wa Yerubaala anatsalako; pakuti anabisala.

6 Pamenepo anasonkhana eni ace onse a ku Sekemu, ndi nyumba yonse ya Milo, namuka namlonga Abimeleki ufumu pa thundu wa coimiritsa ciri m'Sekemu.

7 Ndipo atamuuza Yotamu, anamuka iye naimirira pamutu pa phiri la Gerizimu, nakweza mau ace, napfuula, nanena nao, Mundimvere ine, eni ace a ku Sekemu inu, kuti Mulungu amvere inu.

8 Kumuka inamuka mitengo kudzidzozera mfumu; niti kwa mtengo waazitona, Ukhale iwe mfumu yathu.

9 Koma mtengo waazitona unati kwa iwo, Ngati ndidzasiya kunona kwanga kumene alemekeza nako Mulungu ndi anthu kukalenga pa mitengo?

10 Pamenepo mitengo inati kwa mkuyu. Tiye iwe, ukhale mfumu yathu.

11 Koma mkuyu unanena nao, Ngati ndidzasiya kuzuna kwanga, ndi zipatso zanga zokoma kukalenga pa mitengo?

12 Pamenepo mitengo inati kwa mpesa, Tiye iwe, ukhale mfumu yathu.

13 Koma mpesa unanena nao, Ngati ndidzasiya vinyo wanga wakusekeretsa Mulungu ndi anthu, kukalenga pa mitengo?

14 Pamenepo mitengo yonse inati kwa nkandankhuku, Tiye iwe, ukhale mfumu yathu.

15 Ndipo nkandankhuku unati kwa mitengo, Mukandidzoza mfumu yanu moonadi, tiyeni, thawirani ku mthunzi wanga; mukapanda kutero uturuke mota m'nkandankhuku ndi kunyeketsa mikungudza ya Lebano.

16 Ndipo tsopano, ngati mwacita moona ndi mwangwiro pakulonga Abimeleki ufumu, ngatinso mwamcitira cokoma Yerubaala ndi nyumba yace, ndi kumcitira monga anayenera manja ace;

17 pakuti atate wanga anakugwirirani nkhondo, nataya moyo wace, nakupulumutsani m'dzanja la Amidyani;

18 koma mwaukira nyumba ya atate wanga lero lino, ndi kuwapha ana ace, ndiwo amuna makumi asanu ndi awiri, pa thanthwe limodzi; ndipo mwalonga Abimeleki mwana wa mdzakazi wace, akhale mfumu ya pa eni ace a ku Sekemu, cifukwa ali mbale wanu;

19 ngati tsono mwacitira Yerubaala ndi nyumba yace zoona ndi zangwiro lero lino, kondwerani naye Abimeleki, nayenso akondwere nanu;

20 koma ngati simunatero, uturuke moto kwa Abimeleki, nunyeketse eni ace a ku Sekemu ndi nyumba ya Milo; nuturuke mota kwa eni ace a ku Sekemu, ndi ku nyumba yace ya Milo, nunyeketse Abimeleki.

21 Pamenepo Yotamu anafulumira, nathawa, namuka ku Beeri, nakhala komweko, cifukwa ca Abimeleki mbale wace.

22 Abimeleki atakhala kalonga wa Israyeli zaka zitatu,

23 Mulungu anatumiza mzimu woipa pakati pa Abimeleki ndi eni ace a ku Sekemu; ndi eni ace a ku Sekemu anamcitira Abimeleki mosakhulupirika;

24 kuti ciwawa adacitira ana amuna makumi asanu ndi awiria Yerubaala cimdzere, ndi kuti mwazi wao uikidwe pa mbale wao Abimeleki anawaphayo, ndi pa eni ace a ku Sekemu, amene analimbikitsa manja ace, awaphe abale ace.

25 Ndipo eni ace a ku Sekemu anaika omlalira pamwamba pa mapiri; amene anawawanya onse akudzera njirayi; ndipo anamuuza Abimeleki.

26 Ndipo Gaala, mwana wa Ebedi anadza ndi abale ace, napita ku Sekemu; ndi eni ace a ku Sekemu anamkhulupirira.

27 Ndipo anaturuka kumka kuminda, nachera mphesa m'mindamo, naponda mphesa, napereka nsembe yolemekeza, nalowa m'nyumba ya mulungu wao, nadya, namwa, natemberera Abimeleki.

28 Pamenepo Gaala, mwana wa Ebedi anati, Abimeleki ndani, ndi Sekemu ndani, kuti timtumikire? sindiye mwana wa Yerubaala kodi? ndi Zebuli kazembe wace? Mutumikire amuna a Hamori atate wa Sekemu; koma ameneyo timtumikire cifukwa ninji?

29 Mwenzi anthu awa akadakhala m'dzanja langa; ndikadamcotsadi Abimeleki. Ndipo anati kwa Abimeleki, Curukitsa khamu lako, nuturuke.

30 Pamene Zebuli woyang'anira mudzi anamva mau a Gaala mwana wa Ebedi, anapsa mtima.

31 Natuma mithenga kwa Abimeleki monyenga nati, Taonani Gaala ndi abale ace afika ku Sekemu; ndipo taonani, akupandukitsirani mudzi.

32 Ndipo tsopano, taukani usiku, inu ndi anthu okhala nanu ndi kulalira kuthengo;

33 ndipo kukhale kuti m'mawa, pakuturuka dzuwa, muuke mamawa mugwere mudziwo; ndipo taonani, akakuturukirani iye ndi anthu ali naye, uzimcitira monga lidziwa dzanja lako.

34 Pamenepo Abimeleki anauka ndi anthu onse anali naye, usiku; nalalira a ku Sekemu, magulu anai.

35 Ndipo Gaala mwana wa Ebedi anaturuka, naima polowera pa cipata ca mudzi; nauka Abimeleki ndi anthu anali naye m'molalira.

36 Ndipo pamene Gaala anapenya anthuwo anati kwa Zebuli, Taona, alikutsika anthu kucokera pamwamba pa mapiri, Koma Zebuli ananena naye, Uona mthunzi wa mapiri ndi kuyesa anthu.

37 Koma Gaala ananenanso, nati, Tapenya alikutsika anthu pakati pa dziko, ndi gulu limodzi lidzera olira ya ku thundu wa alauli.

38 Pamenepo Zebuli anati kwa iye, Pakamwa pako mpoti tsopano, muja udanena, Ndani Abimeleki kud timtumikire? awa si anthuwo unawapeputsa? uturuke tsopano, nulimbane nao.

39 Ndipo Gaala anaturuka pamaso pao pa eni ace a ku Sekemu, nalimbana ndi Abimeleki.

40 Koma Abimeleki anampitikitsa, nathawa iye pamaso pace; nagwa olasidwa ambiri mpaka polowera pa cipata.

41 Ndipo Abimeleki anakhala ku Aruma; ndi Zebuli anafngitsa Gaala ndi abale ace kuti asakhale m'Sekemu.

42 Ndipo kunali m'mawa mwace, kuti anthu anaturuka kumka kuminda; ndipo anauza Abimeleki.

43 Pamenepo anatenga anthu, nawagawa magulu atatu, nalalira m'minda; napenya, ndipo taonani, anthu alimkuturuka m'mudzi; nawaukira iye nawakantha.

44 Ndi Abimeleki ndi magulu okhala naye anathamanga naima polowera pa cipata ca mudzi; ndi magulu awiriwo anagwera onse okhala m'munda, nawakantha.

45 Ndipo Abimeleki analimbana ndi mudzi tsiku lija lonse; nalanda mudzi nawapha anthu anali m'mwemo; napasula mudzi; nawazapo mcere.

46 Ndipo pamene eni ace onse a nsanja ya ku Sekemu anacimva, analowa m'ngaka ya nyumba ya Eliberiti.

47 Ndipo anauza Abimeleki kuti amuna onse a nsanja ya ku Sekemu asonkhane.

48 Pamenepo Abimeleki anakwera kumka ku phiri la Zalimoni, iye ndi anthu onse anali naye; natenga nkhwangwa m'dzanja lace Abimeleki, nadula nthambi kumitengo, nainyamula ndi kulika paphewa pace, nati kwa anthu okhala naye, Ici munaciona ndacita, fulumirani, mucite momwemo.

49 Ndi anthu onse anadulanso yense nthambi yace, natsata Abimeleki, naziika pangaka, natentha nazo ngakayo ndi moto; motero anthu onse a nsanja ya ku Sekemu anafanso, amuna ndi akazi ngati cikwi cimodzi.

50 Pamenepo Abimeleki anamuka ku Tebetsi, naumangira Tebetsi misasa, naulanda.

51 Koma m'mudzimo munali nsanja yolimba nathawira kumeneko amuna ndi akazi onse, ndi eni ace onse a mudziwo, nadzitsekereza m'mwemo, nakwera patsindwi pa nsanja.

52 Ndipo Abimeleki anafika kunsania, nalimbana nayo nkhondo, nayandikira kukhomo kwa nsanja, aitenthe ndi moto.

53 Ndipo mkazi wina anaponya mwana wa mphero pamutu pa Abimeleki, naphwanya bade lace.

54 Pamenepo anaitana msanga mnyamata wace wosenza zida zace, nanena naye, Solola lupanga lako nundiphe, angamanenere anthu, ndi kuti, Anamupha ndi mkazi. Nampyoza mnyamata wace, nafa iye.

55 Pamene amuna a Israyeli anaona kuti adafa Abimeleki anamuka yense kumalo kwace.

56 Momwemo Mulungu anambwezera Abimeleki coipaco anacitira atate wace ndi kuwapha abale ace makumi asanu ndi awiri.

57 Ndipo Mulungu anawabwezera coipa conse ca amuna a ku Sekemu pamitu pao, ndipo linawagwera temberero la Yotamu mwana wa Yerubaala.

10

1 Atafa Abimeleki, anauka kupulumutsa Israyeli Tola mwana wa Puwa, mwana wa Dodo munthu wa Isakara; nakhala iye m'Sanriri ku mapiri a Efraimu.

2 Ndipo anaweruza Israyeli zaka makumi awiri ndi zitatu, nafa, naikidwa m'Samiri.

3 Atafa iye, anauka Yairi Mgileadi, naweruza Israyeli zaka makumi awiri mphambu ziwiri.

4 Ndipo anali nao ana amuna makumi atatu okwera pa ana a aburu makumi atatu, iwo ndipo anali nayo midzi makumi atatu, ochedwa midzi ya Yairi, mpaka lero lino, ndiyo m'dziko la Gileadi.

5 Nafa Yairi, naikidwa m'Kamoni.

6 Ndipo ana Israyeli a anaonjeza kucita coipa pamaso pa Yehova, natumikira Abaala, ndi Aastaroti, ndi milungu ya Aramu, ndi milungu ya Sidoni, ndi milungu ya Moabu, ndi milungu ya ana a Amoni, ndi milungu ya Afilisti; ndipo anamleka Yehova osamtumikira.

7 Pamenepo mkwiyo wa Yehova unayakira Israyeli, nawagulitsa m'dzanja la Aftlisti, ndi m'dzanja la ana a Amoni.

8 Ndipo anaphwanya napsinja ana a Israyeli caka ciija, natero ndi ana onse a Israyeli okhala tsidya lija la Yordano m'dziko la Aamori, ndilo Gileadi, zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu.

9 Ndipo ana a Amoni anaoloka Yordano kuthiranso nkhondo Yuda ndi Benjamini, ndi nyumba ya Efraimu; napsinjika kwambiri Israyeli.

10 Ndipo ana a Israyeli anapfuula kwa Yehova ndi kuti, Takucimwirani, popeza tasiya Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.

11 Ndipo Yehova anati kwa ana a Israyeli, Kodi sindinakupulumutsani kwa Aaigupto ndi kwa Aamori, ndi kwa ana a Amoni, ndi kwa Aftlisti?

12 Asidoni omwe, ndi Aamaleki, ndi Amidyani anakupsinjani. Pamenepo munapfuula kwa Ine, ndipo ndinakupulumutsani m'dzanja lao.

13 Koma mwandisiya Ine ndi kutumikira milungu yina, cifukwa cace sindikupulumutsaninso.

14 Mukani ndi kupfuulira kwa milungu munaisankha, ikupulumutseni nyengo ya kusauka kwanu.

15 Koma ana a Israyeli anati kwa Yehova, Tacimwa, muticitire monga mwa zonse zikomera pamaso panu; komatu mutipulumutse lero lino, tikupemphani.

16 Pamenepo anacotsa milungu yacilendo pakati pao, natumikira Yehova; ndipo mtima wace unagwidwa cisoni cifukwa ca mabvuto a Israyeli.

17 Ndipo ana a Amoni analalikiridwa, namanga misasa m'Gileadi. Ndi ana a Israyeli anasonkhana namanga misasa ku Mizipa.

18 Ndipo anthu, akalonga a Gileadi, ananenana wina ndi mnzace, Ndaniyo adzayamba kulimbana ndi ana a Amoni? iye adzakhala mkuru wa onse okhala m'Gileadi.

11

1 Yefita Mgileadi ndipo anali ngwazi yamphamvu, ndiye mwana wa mkazi wadama; koma Gileadi adabala Yefita.

2 Ndipo mkazi wa Gileadi anambalira ana amuna; koma atakula ana amuna a mkaziyo anampitikitsa Yefita, nanena naye, Sudzalandira colowa m'nyumba ya atate wako; pakuti ndiwe mwana wa mkazi wina.

3 Pamenepo Yefita anathawa abale ace, nakhala m'dziko la Tobu; ndipo anyamata opanda pace anasonkhana kwa Yefita, naturuka naye pamodzi.

4 Ndipo kunali, atapita masiku, ana a Amoni anacita nkhondo ndi Israyeli,

5 ndipo kunatero, pamene ana a Amoni anathira nkhondo pa Israyeli, akuru a Gileadi anamuka kutenga Yefita m'dziko la Tobu;

6 nati kwa Yefita, Tiye ukhale kazembe wathu kuti tilimbane ndi ana a Amoni.

7 Ndipo Yefita anati kwa akulu a Gileadi, Simunandida kodi, ndi kundicotsa m'nyumba ya atate wanga? ndipo mundidzeraoji tsopano pokhala muli m'kusauka?

8 Ndipo akuru a Gileadi ananena ndi Yefita, Cifukwa cace cakuti takubwerera tsopano ndico kuti umuke nafe ndi kucita nkhondo ndi ana a Amoni, nudzakhala mkuru wathu wa pa onse okhala m'Gileadi.

9 Ndipo Yefita anati kwa akuru a Gileadi, Mukaodifikitsanso kwathu kucita nkhondo ndi ana a Amoni, nakawapereka Yehova pamaso panga, ndidzakhala mkuru wanu kodi?

10 Ndipo akuru a Gileadi anati kwa Yefita, Yehova ndiye wakumvera pakati pa ife, tikapanda kucita monga momwe wanena.

11 Pamenepo Yefita anamuka ndi akuru a Gileadi, ndipo anthu anamuika mkuru wao ndi mtsogoleri wao; ndipo Yefita ananena mau ace onse pamaso pa Yehova ku Mizipa.

12 Ndipo Yefita anatuma mithenga kwa mfumu ya ana a Amoni, ndi kuti, Ndi ciani ndi Inu, ndi kuti Mwandidzera kuthira nkhondo dziko langa?

13 Ndipo mfumu ya ana a Amoni inati kwa mithenga ya Yefita, Cifukwa Israyeli analanda dziko langa pakukwera iye kucokera ku Aigupto, kuyambira Arinoni mpaka Yaboki, ndi mpaka Yordano; ndipo tsopano uodibwezere maikowa mwamtendere.

14 Ndipo Yefita anatumanso mithenga kwa mfumu ya ana a Amoni;

15 nanena naye, Atero Yefita, Israyeli sanalanda dziko la Moabu kapena dziko la ana a Amoni;

16 pakuti pakukwera iwo kucokera ku Aigupto Israyeli anayenda m'cipululu mpaka Nyanja Yofiira, nafika ku Kadesi;

17 pamenepo Israyeli anatuma mithenga kwa mfumu ya Edomu, ndi kuti, Ndikupemphani ndipitire pakati pa dziko lanu; koma mfumu ya Edomu sinamvera. Natumanso kwa mfumu ya Moabu; nayenso osalola; ndipo Israyeli anakhala m'Kadesi.

18 Pamenepo anayenda m'cipululu, naphazira dziko la Edomu, ndi dziko la Moabu, nadzera kum'mawa kwa dziko la Moabu, namanga misasa tsidya lija la Arinoni; osalowa malire a Moabu, pakuti Arinoni ndi malire a Moabu.

19 Ndipo Israyeli anatuma mithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, mfumu ya ku Hesiboni; nanena naye Israyeli, Tikupemphani tipitire pakati pa dziko lanu, kumka kwathu.

20 Koma Sihoni sanakhulupirira Israyeli kuti apitire pakati pa malire ace; koma Sihoni anamemeza anthu ace onse, namanga misasa ku Yahazi, nathira nkhondo Israyeli.

21 Ndipo Yehova Mulungu wa Israyeli anapereka Sihoni ndi anthu ace onse m'dzanja la Israyeli, ndipo anawakantha, ndi Israyeli analandira colowa cace, dziko lonse la Aamori, nzika za m'dziko lija.

22 Ndipo analandira akhale colowa cao, malire onse a Aamori, kuyambira Arihoni mpaka Yaboki, ndi kuyambira cipululu mpaka Yordano.

23 Motero Yehova Mulungu wa Israyeli anaingitsa Aamori, pamaso pa anthu ace Israyeli, ndipo kodi liyenera kukhala colowa canu?

24 Cimene akulandiritsani Kemosi mulungu wanu, simucilandira colowa canu kodi? Momwemo ali yense Yehova Mulungu wathu waiogitsa pamaso pathu, zacezo tilandira colowa cathu.

25 Ndipo tsopano kodi inu ndinu wabwino woposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Moabu; anatengana konse ndi Israyeli iyeyu kodi, kapena kucita nao nkhondo konse kodi?

26 Pokhala Israyeli m'Hesiboni ndi midzi yace, ndi m'Aroeri ndi midzi yace, ndi m'midzi yonse yokhala m'mphepete mwa Arinoni zaka mazana atatu; munalekeranji kulandanso nthawi ija?

27 Potero sindinakucimwirani ine, koma mundicitira coipa ndinu kundithira nkhondo; Yehova, Woweruzayo, aweruze lero lino pakati pa ana a Israyeli ndi ana a Amoni.

28 Koma mfumu ya ana a Amoni sanamvera mau a Yefita anamtumizirawo.

29 Pamenepo mzimu wa Yehova unamdzera Yefita, napitira iye ku Gileadi, ndi Manase, napitira ku Mizipa wa Gileadi, ndi kucokera ku Mizipa wa Gileadi anapitira kwa ana a Amoni.

30 Ndipo Yefita anawindira Yehova cowinda, nati, Mukaperekatu ana a Amoni m'dzanja langa, ndipo kudzali kuti ciri conse cakuturuka pakhomo pa nyumba yanga kudzakomana nane pakubweranso ine ndi mtendere kucokera kwa ana a Amoni, cidzakhala ca Yehova, ndipo ndidzacipereka nsembe yopsereza.

31

32 Potero Yefita anapita kwa ana a Amoni kuwathira nkhondo; ndipo Yehova anawapereka m'dzanja lace;

33 nawakantha kuyambira ku Aroeri mpaka ufika ku Miniti, ndiyo midzi makumi awiri, ndi ku Abelikerami, makanthidwe akuru ndithu. Motero ana a Amoni anagonjetsedwa pamaso pa ana a Israyeli.

34 Pofika Yefita ku Mizipa ku nyumba yace, taonani, mwana wace wamkazi anaturuka kudzakomana naye ndi malingaka ndi kuthira mang'ombe; ndipo iyeyu anali mwana wace mmodzi yekha, analibe mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.

35 Ndipo kunali, pakumuona anang'amba zobvala zace, nati, Tsoka ine, mwana wanga, wandiweramitsa kwakukuru, ndiwe wa iwo akundisaukitsa ine; pakuti ndamtsegulira Yehova pakamwa panga ine, ndipo sinditha kubwerera.

36 Ndipo anati kwa iye, Atate wanga, mwamtsegulira Yehova pakamwa panu, mundicitire ine monga umo mudaturutsa mau pakamwa panu; popeza Yehova anakucitirani inu cilango pa adani anu, pa ana a Amoni.

37 Ndipo anati kwa atate wace, Andicitire ici, andileke miyezi iwiri, kuti ndicoke ndi kutsikira kumapiri, ndi kulirira unamwali wanga, ine ndi anzanga.

38 Nati iye, Muka. Namuuza amuke akakhale miyezi iwiri; namuka iye ndi anzace, nalirira unamwali wace pamapiri.

39 Ndipo kunali pakutha miyezi iwiri, anabwerera kwa atate wace amene anamcitira monga mwa cowinda cace anaciwinda; ndipo sanamdziwa mwamuna. Motero unali mwambo m'Israyeli,

40 kuti ana akazi a Israyeli akamuka caka ndi caka kumliririra mwana wa Yefita wa ku Gileadi, masiku anai pa caka.

12

1 Pamenepo amuna a Efraimu analalikidwa, napita kumpoto; nati kwa Yefita, Wapitiriraoji kuthira nkhondo ana a Amoni, osatiitana ife timuke nawe? Tidzakutenthera nyumba yako ndimotopamtupako.

2 Ndipo Yefita anati kwa iwo, Ine ndi anthu anga tinatsutsana kwakukuru ndi ana a Amoni, koma pamene ndinakuitanani inu simunandipulumutsa m'dzanju lao.

3 Ndipo pakuona ine kuti simunandipulumutsa, ndinataya moyo wanga ndi kupita kwa ana a Amoni; ndipo Yehova anawapereka m'dzanja langa; mwakwereranji tsono lero lino kundicitira nkhondo?

4 Pamenepo Yefita anamemeza amuna onse a m'Gileadi nalimbana naye Efraimu; ndipo amuna a Gileadi anakantha Efraimu, cifukwa adati, Inu Agileadi ndinu akuthawa Efraimu, pakati pa Efraimu ndi pakati pa Manase.

5 Ndipo Agileadi anatsekereza madooko a Yordano a Efraimu; ndipo kunatero kuti, akati othawa a Efraimu, Ndioloke, amuna a Gileadi anati kwa iye, Ndiwe M-efraimu kodi? Akati, Iai;

6 pamenepo anati kwa iye, Unene tsono Shiboleti; ndipo akati, Siboleti, osakhoza kuchula bwino, amgwira namupha padooko pomwe pa Yordano; ndipo anagwa a Efraimu nthawi ija, zikwi makumi anai mphambu ziwiri.

7 Ndipo Yefita anaweruza Israyeli zaka zisanu ndi cimodzi; nafa Yefita Mgileadi, naikidwa m'mudzi wina wa Gileadi.

8 Ndi pambuyo pace Ibzani wa ku Betelehemu anaweruza Israyeli.

9 Ndipo anali nao ana amuna makumi atatu; ndi ana akazi makumi atatu anawakwatitsa kwina, natengera ana ace amuna ana akazi makumi atatu ocokera kwina. Ndipo anaweruza Israyeli zaka zisanu ndi ziwiri.

10 Nafa Ibzani naikidwa ku Betelehemu.

11 Ndi pambuyo pace Eloni Mzebuloni anaweruza Israyeli; naweruza Israyeli zaka khumi.

12 Nafa Eloni Mzebuloni naikidwa m'Aijaloni m'dziko la Zebuloni.

13 Ndi pambuyo pace Abidonf mwana wa Hilele wa ku Piratoni anaweruza Israyeli.

14 Ndipo anali nao ana amuna makumi anai ndi zidzukulu zazimuna makumi atatu, akuyenda okwera pa ana a aburu makumi asanu ndi awiri; naweruza Israyeli zaka zisanu ndi zitatu.

15 Nafa Abidoni mwana wa Hilele wa ku Piratoni, naikidwa m'Piratoni m'dziko la Efraimu ku mapiri a Amaleki.

13

1 Ndipo ana a Israyeli anaonjeza kucita coipa pamaso pa Yehova; nawapereka Yehova m'dzanja la Afilisti zaka makumi anai.

2 Ndipo panali munthu wina wa Zora wa banja la Adani, dzina lace ndiye Manowa; ndi mkazi wace analibe mwana, sanabala.

3 Ndipo mthenga wa Yehova anamuonekera mkaziyo nanena naye, Taona tsopano, ulibe mwana, wosabala iwe; koma udzaima ndi kubala mwana wamwamuna.

4 Cifukwa cace udzisamalire, usamwe vinyo kapena coledzeretsa, nusadye cinthu ciri conse codetsa;

5 pakuti taona, udzaima, nudzabala mwana wamwamuna; pamutu pace sipadzafika lumo; pakuti mwanayo adzakhalira kwa Mulungu Mnaziri cibadwire; nadzayamba iye kupulumutsa Israyeli m'dzanja la Afilisti.

6 Pamenepo anadza mkaziyo, nanena ndi mwamuna wace ndi kuti, Wandidzera munthu wa Mulungu; maonekedwe ace ndiwo ngati maonekedwe a mthenga wa Mulungu oopsa ndithu; ndipo sindinamfunsa uko acokera kapena sanandiuzanso dzina lace;

7 koma anati kwa ine, Taona, udzaima, ndi kubala mwana wamwamuna; ndipo tsopano usamwe vinyo kapena coledzeretsa, nusadye ciri conse codetsa; pakuti mwanayo adzakhalira kwa Mulungu Mnaziri cibadwire mpaka tsiku la kufa kwace.

8 Pamenepo Manowa anapembedza Yehova, nati, Yehova, ndikupemphani, atidzerenso munthu wa Mulungu mudamtumayo, natilangize ico tizicitira mwanayo akadzabadwa.

9 Ndipo Mulungu anamvera mau a Manowa; ndi mthenga wa Mulungu anamdzeranso mkaziyo, pamene anali m'munda, mwanuna wace Manowa palibe.

10 Ndipo mkaziyo anafulumira nathamanga, nauza mwamuna wace, nanena naye, Taona, wandionekera munthu anandidzerayo tsiku lija.

11 Nanyamuka Manowa natsata mkazi wace, namdzera mwamuna uja, nanena naye, Kodi ndinu mwamuna ujamunalankhulandimkaziyu? Ndipo anati, Ndine amene.

12 Nati Manowa, Acitike tsopano mau anu; koma makhalidwe ace a mwanayo ndi macitidwe ace adzatani?

13 Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa Manowa, Zonse ndinazinena ndi mkazi azisamalire.

14 Ciri conse cicokera kumpesa asadyeko, asamwe vinyo kapena coledzeretsa, kapena kudya ciri conse codetsa; zonse ndinamlamulira azisunge.

15 Ndipo Manowa anati kwa mthenga wa Yehova, Tiloleni tikucedwetseni kuti tikukonzereni mwana wa mbuzi.

16 Koma mthenga wa Yehova anati kwa Manowa, Ungakhale undicedwetsa, sindidzadya mkate wako; ndipo ukakonza nsembe yopsereza, uziipereka kwa Yehova. Pakuti Manowa sanadziwa kuti ndiye mthenga wa Yehova.

17 Ndipo Manowa anati kwa mthenga wa Yehova, Dzina lanu ndani, kuti, atacitika mau anu, tikucitireni ulemu.

18 Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa iye, Ufunsiranji dzina langa, popeza liri lodabwitsa?

19 Pamenepo Manowa anatenga mwana wa mbuzi pamodzi ndi nsembe yaufa, nazipereka kwa Yehova pathanthwe; ndipo mthengayo anacita modabwitsa, ndi Manowa ndi mkazi wace ali cipenyereo

20 Pakuti kunali, pakukwera lawi la mota pa guwa la nsembe kumwamba, mthenga wa Yehova anakwera m'lawi la pa guwalo; ndi Manowa ndi mkazi wace ali cipenyere; nagwa iwowa nkhope zao pansi.

21 Ndipo mthenga wa Yehova sanaonekeranso kwa Manowa kapena kwa mkazi wace. Pamenepo anadziwa Manowa kuti ndiye mthenga wa Yehova.

22 Nati Manowa kwa mkazi wace, Tidzafa ndithu pakuti taona Mulungu.

23 Koma mkazi wace ananena naye, Yehova akadafuna kutipha, sakadalandira nsembe yopsereza ndi nsembe yaufa pa dzanja lathu, kapena kutionetsa izi zonse, kapena kutimvetsa zoterezi nthawi yino.

24 Ndipo mkaziyo anabala mwana wamwamuna namucha dzina lace Samsoni; nakula mwanayo, Yehova namdalitsa.

25 Ndipo mzimu wa Yehova unayamba kumfulumiza mtima ku misasa ya Dani pakati pa Zora ndi Esitaoli.

14

1 Ndipo Samsoni anatsikira ku Timna, naona mkazi wa ku Timna wa ana akazi a Afilisti.

2 Nakwera iye, nauzaatatewacendi amai wace, nati, Ndapenya mkazi m'Timna wa ana akazi a Afilisti; ndipo tsono munditengere uyu akhale mkazi wanga.

3 Koma atate wace ndi amai wace ananena naye, Kodi palibe mkazi mwa ana akazi a abale ako, kapena mwa anthu a mtundu wanga onse, kuti wamuka kutenga mkazi wa Afilisti osadulidwawo? Nati Samsoni kwa atate wace, Nditengereni iye, pakuti andikonda pamaso panga.

4 Koma atate wace ndi amai wace sanadziwa kuti cidacokera kwa Yehova ici; popeza analikufuna kutola cifukwa ndi Afilisti. Ndipo nthawi ija Afilisti analamulira Israyeli.

5 Pamenepo anatsikira Samsoni, ndi atate wace ndi mai wace ku Timna, nadza ku minda yamphesa ya Timna; ndipo taona, mwana wa mkango wakomana naye namdzumira.

6 Ndipo unamgwera iye kolimba mzimu wa Yehova, naung'amba monga akadang'amba mwana wa mbuzi, wopandakanthu m'dzanjaliace; koma sanauza atate wace kapena amai wace cimene adacicita.

7 Ndipo anatsika nakamba ndi mkazi, namkonda Samsoni pamaso pace.

8 Atapita masiku ndipo anabweranso kudzamtenga, napambuka iye kukaona mtembo wa mkango; ndipo taona, m'citanda ca mkango munali njuci zoundana, ndi uci.

9 Ndipo anaufula ndi dzanja lace, nayenda, namadya alimkuyenda, nadza kwa atate wace ndi amai wace, nawapatsa, nadya iwo; koma sanawauza kuti adaufula uciwo m'citanda ca mkango.

10 Ndipo atate wace anatsikira kwa mkazi; ndi Samsoni anakonzerapo madyerero; pakuti amatero anyamata.

11 Ndipo kunali, pamene anamuona, anabwera nao anzace makumi atatu akhale naye.

12 Nanena nao Samsoni, Mundilole ndikuphereni mwambi; mukanditanthauziratu uwu m'masiku asanuwa a madyerero, ndi kuukumika uwu, ndidzakupatsani malaya a nsaru yabafuta makumi atatu, ndi zobvala zosinthanitsa makumi atatu;

13 koma ngati simukhoza kunditanthauzira uwu mudzandipatsa ndinu Malaya a nsaru yabafuta makumi atatu ndi zobvala zosinthanitsa makumi atatu. Pamenepo ananena naye, Mwambi wako tiumve.

14 Ndipo ananena nao, Cakudya cinaturuka m'mwini kudya, Ndi cozuna cinaturuka m'mwini mphamvu, Ndipo masiku atatu sanakhoza kutanthauzira mwambiwo.

15 Koma kunali, tsiku lacisanu ndi ciwiri anati kwa mkazi wa Samsoni, Kopa mwamuna wako, atitanthauzire mwambiwo; tingatenthe iwe ndi nyumba ya atate wako ndi mota. Kodi mwatiitana kulanda zathu; si momwemo?

16 Ndipo mkazi wa Samsoni analira pamaso pace, nati, Ungondida, osandikonda; waphera anthu a mtundu wanga mwambi, osanditanthauzira ine. Ndipo ananena naye, Taona, sindinatanthauzira atate wanga kapena amai wanga, kodi ndikutanthauzire iwe?

17 Ndipo analira pamaso pace masiku asanu ndi awiriwo pocitika madyerero ao; koma kunali kuti tsiku lacisanu ndi ciwiri anamuuza, popeza anamuumiriza; ndipo anatanthauzira anthu a mtundu wace mwambiwo.

18 Ndipo amuna a pamudzi anati kwa Samsoni tsiku lacisanu ndi ciwiri, lisanalowe dzuwa, Cozuna coposa uci nciani; ndi camphamvu coposa mkango nciani? Pamenepo ananena nao, Mukadapanda kulima ndimthandi wanga, Simukadakumika mwambi wanga.

19 Ndipo mzimu wa Yehova unamgwera Samsoni, natsikira iye kwa Asikeloni, nawakantha amuna makumi atatu, natenga zobvala zao, nawapatsa okumika mwambiwo zobvala zosinthanitsa. Koma adapsa mtima, nakwera kumka ku nyumba ya atate wace.

20 Ndipo mkazi wace wa Samsoni anakhala wa mnzace, amene adakhala bwenzi lace.

15

1 Ndipo kunali atapita masiku, nyengo ya kuceka tirigu Samsoni anakaceza ndi mkazi wace ndi kumtengera mbuzi, nati, Ndidzalowa kwa mkazi wanga kucipinda. Koma atate wace sanamlola kulowamo.

2 Nati atate wace, Ndinanenetsa kuti umuda konse, potero ndinampereka kwa bwenzi tako; mng'ono wace sakoma koposa iye nanga? ukhale naye, m'malo mwa winayu.

3 Koma Samsoni ananena nao, Nthawi yino ndikhala wosaparamula pa Afilisti, powacitira coipa ine.

4 Namuka Samsoni, nagwira ankhandwe mazana atatu, natenga miuni, nalunza micira, naika muuni pakati pa micira iwiri iri yonse.

5 Nayatsa miuni, nawataya ku tirigu wosaceka wa Afilisti, natentha miulu ndi tirigu wosaceka yemwe, ndi minda ya azitona yomwe.

6 Pamenepo Afilisti anati, Wacita ici ndani? Nati, Samsoni mkamwini wa munthuyo wa ku Timna, popeza analanda mkazi wace, nampereka kwa mnzace. Pamenepo Afilisti anakwera namtentha mkaziyo ndi atate wace ndi moto.

7 Ndipo Samsoni ananena nao, Mukatero ndidzakubwezerani cilango ndi pamenepo ndidzaleka.

8 Ndipo anawakantha nyung'unyu ndi ncafu, makanthidwe akuru; natsika nakhala m'phanga mwa thanthwe la ku Etamu.

9 Pamenepo Afilisti anakwera, namanga misasa m'Yuda, natandika m'Leki

10 Ndipo anthu a Yuda anati, Mwatikwerera cifukwa ninji? Nati iwo, Takwera kumanga Samsoni, kumcitira iye monga anaticitira ife.

11 Pamenepo anatsikira ku phanga la Etamu amuna zikwi zitatu, nati kwa Samsoni, Sudziwa kodi kuti Atilisti ndiwo akutilamulira ife? nciani ici waticitira? Nati iye kwa iwowa, Monga anandicitira ine ndawacitira iwo.

12 Ndipo ananena naye, Tatsika ife tikumange, kuti tikupereke m'dzanja la Atilisti. Nanena nao Samsoni, Mundilumbirire kuti simudzandigwera nokha.

13 Ndipo anati kwa iye, Iai, koma kumanga tidzakumanga, ndi kukupereka m'dzanja lao; koma kupha sitikupha iwe. Nammanga iye ndi zingwe ziwiri zatsopano, nakwera naye kucokera kuthanthwe.

14 Pamene anafika ku Leki Afilisti anapfuula pokomana naye; koma mzimu wa Yehova unamgwera kolimba, ndi zingwe zokhala pa manja ace zinanga bwazi lopserera ndi moto, ndi zomangira zace zinanyotsoka pa manja ace.

15 Ndipo anapeza cibwano catsopano ca buru, natambasula dzanja lace nacigwira, nakantha naco amuna cikwi cimodzi.

16 Nati Samsoni, Ndi cibwano ca buru, miuru miuru, Amuna cikwi ndawakantha ndi cibwano ca buru.

17 Ndipo kunali, atatha kunena, anataya cibwano m'dzanja lace; nawacha maiowo Ramati-leki ndiko kunena citunda ca cibwano.

18 Ndipo anamva ludzu lambiri, naitana kwa Yehova, nati, Mwapatsa Inu cipulumutso ici cacikuru ndi dzanja la kapolo wanu; ndipo kodi ndife nalo ludzu tsopano ndi kugwa m'dzanja la osadulidwa awa?

19 Pamenepo Mulungu anang'amba pokumbika paja pit Leki, naturukamo madzi; namwa iye, nubwera moyo wace, natsitsimuka iye; cifukwa cace anawacha dzina lace, Kasupe wa wopfuula, ndiwo m'Leki mpaka lero lino.

20 Ndipo Samsoni anaweruza Israyeli m'masiku a Afilisti zaka makumi awiri.

16

1 Ndipo Samsoni anamuka ku Gaza, naonako mkazi wadama, nalowana naye.

2 Koma wina anauza a ku Gala, ndi kuti, Samsoni walowa kuno. Pamenepo anamzinga, namlalira usiku wonse pa cipata ca mudzi, nakhala cete usiku wonse ndi kuti, Tidikire mpaka kuca, pamenepo tidzamupha,

3 Koma Samsoni anagona mpaka pakati pa usiku, nauka pakati pa usiku, nagwira zitseko za pa cipata ca mudzi, ndi mphuthu ziwirizo, nazicotsa ndi mpiringidzo womwe, naziika pa mapewa ace, nakwera nazo pamwamba pa phiri liri pandunji pa Hebroni.

4 Ndipo pambuyo pace kunali kud anakonda mkazi m'cigwa ca Soreki, dzina lace ndiye Delila.

5 Ndipo akalonga a Atilisti anamkwerera mkaziyo, nanena naye, Umkope nuone umo mucokera mphamvu yace yaikuru, ndi umo tingakhoze kumtha khama, kuti timmange kumzunza; ndipo tidzakupatsa ali yense ndalama mazana khumi ndi limodzi.

6 Pamenepo Delila anati kwa Samsoni, Ndikupempha, undiuze umo mucokera mphamvu yako yaikuru, ndi cimene angakumange naco, kuti akuzunze.

7 Nanena naye Samsoni, Akandimanga nazo nsinga zatsopano zisanu ndi ziwiri zosauma, ndidzakhala wofoka, wakunga munthu wina.

8 Pamenepo akalonga a Afilisti anakwera nazo kwa mkaziyo nsinga zatsopano zisanu ndi ziwiri zosauma; ndipo iye anammanga nazo.

9 Koma anali nao omlalira m'cipinda ca m'kati. Nanena naye, Afilisti akugwera, Samsoni, Pamenepo anadula nsingazi, monga iduka nkhosi ya bwazi pokhudza moto. M'mwemo mphamvu yace siinadziwike.

10 Pamenepo Delila anati kwa Samsoni, Taona, wandipusitsa, ndi kundiuza mabodza; undiuze tsopano, ndikupempha, cimene angakumange naco.

11 Nanena naye, Akandimangitsa nazo zingwe zatsopano, zosagwira nazo nchito pamenepo ndidzakhala: wofoka wakunga munthu wina.

12 Ndipo Delila anatenga nsinga zatsopano, nammanga nazo, nanena naye, Atilisti akugwera, Samsoni. Ndi omlalira analikulinda m'cipinda ca m'kati. Koma anazidula pa manja ace ngati thonje.

13 Pamenepo Delila anati kwa Samsoni, Mpaka tsopano wandipusitsa, ndi kundiuza mabodza; undiuze cimene angakumange naco. Nanena naye, Ukaomba njombi zisanu ndi ziwiri za pamutu panga mwa thonje loyala ndiko.

14 Ndipo anacimanga ndi phanga, nati kwa iye, Akugwera Afilisti, Samsoni; nagalamuka iye patulo tace, nazula phanga la pamtanda, ndi thonje loyala lomwe.

15 Pamenepo ananena naye, Ukati bwanji, Ndikukonda, osamvana nane mtima wako? wandipusitsa katatu tsopano, osandiuza umo mucokera mphamvu yako yaikuru,

16 Ndipo kunali, popeza anamuumiriza masiku onse ndi mau ace, oamkakamiza, moyo wace unabvutika nkufuna kufa.

17 Pomwepo anamfotokozera mtima wace wonse, nanena naye, Pamutu panga sipanapite lumo, pakuti ndine Mnaziri wa Mulungu ciyambire mimba ya mai wanga; akandimeta, mphamvu yanga idzandicokera, ndidzakhala wofoka wakunga munthu wina ali yense.

18 Ndipo pamene Delila anaona kuti adamfotokozera mtima wace wonse, anatuma naitana akalonga a Afilisti, ndi kuti, Kwerani nthawi yino, pakuti wandifotokozera za mtima wace wonse. Nakwera akalonga a Afilisti nadza kwa iye nabwera nazo ndalamazo m'dzanja lao.

19 Pamenepo anamgonetsa pa mabondo ace, naitana munthu, nameta njombi zace zisanu ndi ziwiri; nayamba kumzunza, nimcokera mphamvu yaceo

20 Ndipo anati, Afilisti akugwera, Samsoni. Nagalamuka iye m'tulo tace, nati, Ndizituruka ngati nthawi zina, ndi kudzitakasika. Koma sanadziwa kuti Yehova adamcokera.

21 Pamenepo Afilisti anamgwira, namkolowola maso, natsika naye ku Gaza, nammanga ndi maunyolo amkuwa; namperetsa m'kaidi.

22 Koma atammeta tsitsi la pamutu pace linayamba kumeranso.

23 Ndipo anasonkhana akalonga a Afilisti kuperekera Dagoni mulungu wao nsembe yaikuru, ndi kusekerera; pakuti anati, Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu m'dzanja lathu.

24 Ndipo pakumuona anthu analemekeza mulungu wao, pakuti anati, Mulungu wathu wapereka m'dzanja lathu mdani wathu, ndiye wakupasula dziko lathu, amene anatiphera ambiri.

25 Ndipo kunali, pakukondwera mitima yao, anati, Kaitaneni Samsoni, atisewerere. Naitana Samsoni m'kaidi; nasewera iye pamaso pao; ndipo anamuika iye pakati pa mizati.

26 Ndipo Samsoni anati kwa mnyamata womgwira dzanja, Ndileke, ndikhudze mizati imene nyumba ikhazikikapo, kuti nditsamirepo.

27 Koma nyumbayi inadzala ndi amuna ndi akazi; ndi akalonga onse a Afilisti anali momwemo ndi patsindwi panali amuna ndi akazi ngati zikwi zitatu akuyang'ana pakusewera Samsoni.

28 Pamenepo Samsoni anaitana kwa Yehova, nati, Yehova, Mulungu, dikupempha mundikumbukile, ndikupemphani, ndi kundilimbitsa, ndikupemphani, nthawi yino yokha, Mulungu, kuti ndidzilipsiriretu tsopano apa Afilisti, cifukwa ca maso anga awiri.

29 Ndipo Samsoni anagwira mizati iwiri ya pakati imene nyumba inakhazikikapo, natsamirapo wina ndi dzanja lamanja, ndi unzace ndi dzanja lamanzere.

30 Nati Samsoni, Ndife nao Afilisti; nadziweramira mwamphamvu; ndipo nyumba idagwa pa akalonga, ndi pa anthu onse anali m'mwemo. Motero akufa amene anawapha pa kufa kwace anaposa amene anawapha akali moyo.

31 Pamenepo anatsika abale ace ndi banja lonse la atate wace, namnyamula, Dakwera naye, namuika pakati pa Zora ndi Esitaoli, m'manda a Manowa atate wace. Ndipo adaweruza Israyeli zaka makumi awiri.

17

1 Ndipo ku mapiri a Efraimu kunali munthu dzina lace ndiye Mika.

2 Ndipo iye anati kwa amai wace, Ndarama zija mazana khumi ndi limodzi anakuberani zimene munatembererapo, ndi kunenanso m'makutu mwanga, taonani ndaramazo ndiri nazo, ndinazitenga ndine. Pamenepo amai wace anati, Yehova adalitse mwana wanga.

3 Nabwezera amace ndarama zija mazana khumi ndi limodzi; nati amai wace, Kupatula ndapatulira Yehova ndaramazo zicoke ku dzanja langa, zimuke kwa mwana wanga, kupanga nazo dikupempha fano losema ndi fane loyenga; m'mwemo ndikubwezera izi.

4 Ndipo pamene anambwezera mai wace ndaramazo, mai wace anatapako ndarama mazana awiri, nazipereka kwa woyenga, ndiye anazipanga fane losema ndi fano loyenga; ndipo linakhala m'nyumba ya Mika.

5 Koma munthuyu Mika anali nayo nyumba ya milungu, napanga cobvala ca wansembe, ndi timafano, namninkha zansembe mwana wace wina wamwamuna, amene anakhala wansembe wace.

6 Masikuwa panalibe mfumu m'Israyeli, yense anacita comuyenera m'maso mwace.

7 Ndipo panali mnyamata wa ku Betelehemu-Yuda wa banja la Yuda, ndiye Mlevi, nagonera iye komweko.

8 Adacokera munthuyo m'mudzi m'Betelehemu-Yuda, kugonera pali ponse akapeza pokhala; ndi pa ulendo wace anafika ku mapiri a Efraimu, ku nyumba ya Mika.

9 Ndipo Mika ananena naye, Ufumira kuti? Nati kwa iye, Ndine Mlevi wa ku Betelehemu-Yuda, ndirikumuka kugonera kumene ndikapeza pokhala.

10 Nanena naye Mika, Khalitsa nane, nukhale atate wanga, ndi wansembe wanga, ndipo ndidzakupatsa ndarama khumi pacaka, ndi cobvala cofikira, ndi zakudya zako. Nalowa Mleviyo.

11 Ndi Mleviyo anabvomera kukhalitsa ndi munthuyo; ndi mnyamatayo anamkhalira ngati mmodzi wa ana ace.

12 Ndipo Mika anamninkha zansembe Mleviyo, ndi mnyamatayo anakhala wansembe wace, nakhala m'nyumba ya Mika.

13 Nati Mika, Tsopano ndidziwa kuti Yehova adzandicitira cokoma, popeza ndiri naye Mlevi akhale wansembe wanga.

18

1 Masiku ajawo panalibe mfumu m'Israyeli; masiku ajanso pfuko la Adani anadzifunira colowa cakukhalako; pakuti kufikira tsiku lija sicinawagwera colowa cao pakati pa mapfuko a Israyeli.

2 Ndipo ana a Dani anatuma a banja lao amuna asanu a mwa iwo onse, anthu olimba mtima, a ku Zora, ndi a ku Esitaoli, a kuzonda dziko ndi kufunafunamo; nanena nao, Mukani, mufunefune m'dziko. Nafika iwo ku mapiri a Efraimu ku nyumba ya Mika, nagona komweko,

3 Pokhala iwo m'nyumba ya Mika, anazindikira mau a mnyamata Mleviyo, napambukirako, nanena naye, Anadza nawe kuno ndani? ucitanji muno? ukhala naco ciani kuno?

4 Ndipo ananena nao, Mika anandicitira cakuti cakuti, napangana nane za nchito, ndipo ndikhala wansembe wace.

5 Pamenepo ananena naye, Utifunsire kwa Mulungu, kuti tidziwe ngati ulendo wathu timukawo udzakoma.

6 Nanena nao wansembeyo, Mukani mumtendere, ulendo wanu muyendawo uli pamaso pa Yehova.

7 Pamenepo amuna asanuwa anacoka, nafika ku Laisi; naona anthu anali m'mwemo, kuti anakhalaokhazikika mtima, monga anakhala Asidoni, odekha ndi osatekeseka; popeza m'dzikomo munalibe mwini bwalo wakudtitsa manyazi m'cinthu ciri conse; nasiyana kutali ndi Asidoni, ndipo analibe kanthu ndi munthu ali yense.

8 Ndipo asanuwo anafikanso kwa abale ao ku Zora ndi Esitaoli; ndi abale ao ananena nao, Mutani inu?

9 Nati iwo, Taukani, tiwakwerere; pakuti tapenya dziko, ndipo taonani, ndilo lokoma ndithu; ndi inu muli cete kodi? musamacita ulesi kumuka ndi kulowa kulandira dzikolo,

10 Pomuka inu mudzafikira anthu okhazikika mtima ndi dziko ladtando; pakuti Mulungu walipereka m'dzanja lanu; pamenepo mposasowa kanthu kali konse kali pa dziko lapansi.

11 Pamenepo amuna mazana asanu ndi limodzi, omangira zida za nkhondo m'cuuno, anaphumulako a banja la a Dani, anacokera ku Zora, ndi ku Esitaoli.

12 Nakwera namanga misasa m'Kiriyati-yearimu, m'Yuda; cifukwa cace anacha dzina lace la malowo cigono ca Dani, mpaka lero; taona, ali m'tseri mwa Kiriyatiyearimu.

13 Ndipo anapiririra komweko kumka ku mapiri a Efraimu, nadza ku nyumba ya Mika.

14 Pamenepo anayankha amuna asanu anamukawo kukazonda dziko la Laisi, nanena ndi abale ao, Kodi mudziwa kuti m'nyumba izi muli cobvala ca wansembe, ndi timafano ndi fano losema, ndi fano loyenga? Ndipo tsopano dziwani coyenera inu kucita.

15 Napambuka iwo kumkako, nafika ku nyumba ya mnyamata Mleviyo, ndiyo nyumba ya Mika, namfunsa ngati ali bwanji.

16 Ndipo amuna mazana asanu ndi limodzi omangira zida zao za nkhondo m'cuuno, ndiwo a ana a-Dani, analikuima polowera pa cipata;

17 koma amuna asanu omukawo kukazonda dziko anakwera nalowako, natenga fano losema, ndi cobvala ca wansembe ndi timafano, ndi fano loyenga; ndi wansembe anaima polowera pa cipata pamodzi ndi amuna mazana asanu ndi limodzi omangira zida za nkhondo m'cuuno.

18 Atalowa iwo m'nyumba ya Mika, natengako fane losema, cobvala ca wansembe, ndi timafano, ndi fano loyenga, wansembeyo ananena nao, Mucitanji?

19 Ndipo ananena naye, Khala cete, tseka pakamwa pako, numuke nafe, nutikhalire atate ndi wansembe wathu; cikukomera nciti, kukhala wansembe wa nyumba ya munthu mmodzi, kapena kukhala wansembe wa pfuko ndi banja m'Israyeli?

20 Nukondwera mtima wa wansembeyo, natenga iye cobvala ca wansembe, ndi timafano ndi fano losema, nalowa pakati pa anthu.

21 Atatero anabwerera, nacoka, natsogoza ana ang'ono ndi zoweta ndi akatundu.

22 Atafika kutari ndi nyumba ya Mika, Mikayo anawamemeza amuna a m'nyumba zoyandikizana ndi yace, natsata ndi kuwapeza ana a Dani.

23 Ndipo anapfuula kwa ana a Dani. Naceuka iwo nati kwa Mika, Cakusowa ciani, kuti wamemeza anthu ako?

24 Nati iye, Mwanditengera milungu yanga ndinaipanga, ndi wansembe, ndi kucoka; cinditsaliranso ciani? ndipo muneneranji kwa ine, Cakusowa nciani?

25 Koma ana a Dani anati kwa iye, Mau ako asamveke ndi ife, angakugwere anthu owawa mtima, nukataya moyo wako ndi wa iwo a m'nyumba mwako.

26 Nayenda ulendo wao ana a Dani; ndipo Mika pakuona kuti anamposa mphamvu, anatembenuka nabwerera kunyumba kwace.

27 M'mwemo anatenga zimene Mika adacipanga, ndi wansembe anali naye, nafika ku Laisi, kwa anthu odekha ndi okhazikika mtima, nawakantha ndi lupanga lakuthwa, natentha mudzi wao ndi moto.

28 Ndipo panalibe wolanditsa, popeza ku Sidoni nkutali, ndipo analibe kuyenderana ndi anthu ena; ndiko ku cigwa cokhala ku Betirehobo. Pamenepo anamanganso mudziwo, nakhala m'mwemo.

29 Ndipo analicha dzina la mudziwo Dani, kutsata dzina la atate wao Dani wombala Israyeli; koma poyambapo dzina la mudzi linali Laisi.

30 Ndipo ana a Dani anadziimitsira fane losemalo; ndi Yonatani mwana wa Gerisomu mwana wa Manase, iye ndi ana ace amuna anali ansembe a pfuko la Adani mpaka tsiku lija anatenga ndende anthu a m'dziko.

31 Motero anadziikira fane losema la Mika, limene adalipanga, masiku onse okhala nyumba ya Mulungu ku Silo.

19

1 Ndipo kunali, masiku aja, pamene panalibe mfumu m'Israyeli, panali munthu Mlevi wogonera kutseri kwa mapiri a Efraimu amene anadzitengera mkazi wamng'ono wa ku Betelehemu-Yuda.

2 Koma mkazi wace wamng'ono anacita cigololo akali naye, namcokera kumka ku nyumba ya atate wace ku Betelehemu-Yuda, nakhalako nthawi ya miyezi inai.

3 Koma anauka mwamuna wace namtsata kukamba naye zamtima, kumbwezanso; napita ndi mnyamata wace, ndi aburu awiri. Ndipo mkaziyo anadza naye ku nyumba ya atate wace. Ndipo pakumuona atate wa mkaziyo, anakondwera kukomana naye.

4 Ndipo mpongozi wace, ndiye atate wa mkaziyo, anamuimika kuti akhale naye masiku atatu; nadya namwa nagona komweko.

5 Ndipo kunali, tsiku lacinai, analawirira mamawa, nanyamuka iye kucoka; koma atate wa mkaziyo anati kwa mkamwini wace, Limbitsa mtima wako ndi mkate pang'ono, ndipo utatero upite.

6 Nakhala pansi nadya namwa onse awiri pamodzi; nati kwa munthuyo atate wa mkaziyo, Ubvomere, ugone kuno usiku, nusekerere mtima wako.

7 Ndipo munthuyo ananyamuka kuti amuke; koma mpongozi waceyo anamkakamiza, nagonanso komweko.

8 Nalawirira mamawa tsiku lacisanu kuti amuke, koma atate wa mkaziyo anati, Ulimbitse mtima wako, nulindire lipendeke dzuwa; nadya iwo onse awiri.

9 Pamenepo munthuyo ananyamuka kucoka, iye ndi mkazi wace wamng'ono ndi mnyamata wace; koma mpongozi wace, atate wa mkaziyo, ananena naye, Tapenya, lapendeka dzuwa, ugone kuno usiku; tapenya lapendekatu dzuwa, ugone kuno, nusekerere mtima wako; nimulawire mamawa kumka ulendo wanu kwanu.

10 Koma munthuyo anakana kugonako usiku, nanyamuka, nacoka, nadza pandunji pa Yebusi (ndiwo Yerusalemu); ndi pamodzi naye panali aburu awiri omangirira mbereko; anali nayenso mkazi wace wamng'ono.

11 Pofika iwo pa Yebusi linalimkulowa dzuwa, ndi mnyamata anati kwa mbuye wace, Tiyeni, tipambukire mudzi uwu wa Ayebusi ndi kugona pomwepa.

12 Koma mbuye wace ananena naye, Tisapambukire mudzi wacilendo, wosati wa ana a lsrayeli, koma tipitirire kumka ku Gibeya,

13 Nati kwa mnyamata wace, Tiyeni, tiyandikire kwinako: tigone m'Gibeya, kapena m'Rama.

14 Napitiriraiwo, nayenda, ndi dzuwa linawalowera pafupi pa Gibeya, ndiwo wa Benjamini.

15 Napambukirako, kuti alowe nagone ku Gibeya; nalowa iye, nakhala pansi m'khwalala la mudziwo, pakuti panalibe wina wowalandira m'nyumba agonemo, wakuwapatsa pogona.

16 Ndipo taonani, munthu nkhalamba anacokera ku nchito yace kumunda madzulo; munthuyu ndiye wa ku mapiri a Efraimu, nagonera ku Gibeya; kuma anthu pamenepo ndiwo Abenjamini.

17 Pamene anakweza maso ace anaona munthu wa pa ulendoyo m'khwalala la mudzi; ndi nkhalambayo inati, Umuka kuti? ufumira kuti?

18 Ndipo ananena nayo, Tirikucokera ku BetelehemuYuda, kumka ku mbali za mapiri a Efraimu, ndiko ndifumira ine; koma ndidamuka ku Betelehemu-Yuda; ndipo tsopano ndiri kumuka ku nyumba ya Yehova; koma palibe munthu wondipatsa nyumba.

19 Ngakhale maudzu ndi cakudya ca aburu athu ziriko; ndi mkate ndi vinyo zirikonso kwa ine ndi kwa mdzakazi wako ndi kwa mnyamata wokhala ndi aka polo ako; kosasowa kanthu.

20 Ndipo nkhalambayo inati, Mtendere ukhale ndi iwe, komatu, zosowa zako zonse ndidzakuparsa ndi ine; pokhapo usa gone m'khwalala.

21 Pamenepo anamlonga m'nyumba yace, napatsa aburu cakudya; ndipo iwo anasamba mapazi ao, nadya, namwa.

22 Pokondweretsa iwo mitima yao, taonani amuna a m'mudziwo, ndiwo anthu otama zopanda pace, anazinga nyumba, nagogodagogoda pacitseko; nati kwa mwini nyumba nkhalambayo ndi kuti, Turutsa mwamunayo adalowa m'nyumba mwako kuti timdziwe.

23 Ndipo munthu mwini nyumba anawaturukira nanena nao, lai, abale anga, musacite coipa cotere; popeza mwamuna uyu walowa m'nyumba mwanga, musacite copusa ici.

24 Taonani, mwana wanga wamkazi ndiye namwali, ndi mkazi wace wamng'onoyo siwa; ndiwaturutse iwo, muwacepetse iwo, ndi kuwacitira monga muyesa cokoma; koma mwamuna uyu musamcitire copusa ici.

25 Koma amunawo sanafuna kumvera; motero munthuyu anagwira mkazi wace wamng'ono, naturuka naye kwa iwo kunja; namdziwa iwo, nacita naye zoipa usiku wonse mpaka m'mawa; namlola acoke mbandakuca.

26 Nadza mkaziyo kutaca, nagwa pakhomo pa nyumba ya munthu padali mbuye wace, kufikira kutayera.

27 Pamene mbuye wace anauka mamawa, natsegula pakhomo pa nyumba, naturuka kumka ulendo wace, taona, mkazi wace wamng'onoyo, atagwa pakhomo pa nyumba ndi manja ace paciundo.

28 Ndipo ananena naye, Tauka, timuke; koma panalibe womyankha. Pamenepo anamuika pa buru; nanyamuka mwamunayo, namka kwao.

29 Ndipo pofika iye kunyumba kwace, anatenga mpeni, nagwira mkazi wace wamng'onoyo namgawa ciwalo ciwalo magawo khumi ndi awiri, namtumiza ku mame onse a Israyeli.

30 Ndipo kunali kuti onse amene anaciona anati, Sicinacitika, inde sicinaoneka cotere ciyambire tsiku lokwera ana a Israyeli kuturuka m'dziko la Aigupto mpaka lero lino; lingiriranipo, mupangane nzeru, nimunene.

20

1 Pamenepo anaturuka ana onse a Israyeli, nuunjikana msonkhano kwa Yehova ku Mizipa ngati munthu mmodzi, kuyambira ku Dani mpaka Beereseba ndi dziko la Gileadi lomwe.

2 Ndipo akuru a anthu onse a mapfuko onse a Israyeli anadziimika mu msonkhano wa anthu a Mulungu, anthu oyenda pansi zikwi mazana anai akusolola lupanga,

3 Ndipo ana a Benjamini anamva kuti ana a Israyeli adakwera kumka ku Mizipa, Nati ana a Israyeli, Nenani, coipa ici cinacitika bwanji?

4 Ndipo Mlevi, mwamuna wa mkazi anaphedwayo, anayankha nati, Ndinadza ine ku Gibeya wa Benjamini, ine ndi mkazi wanga wamng'ono, kugonako.

5 Nandiukira eni ace a Gibeya, nandizingira nyumba usiku; nafuna kundipha ine, namcitira coipa mkazi wanga wamng'ono, nafa iye,

6 Pamenepo ndinagwira mkazi wanga wamng'ono ndi kumgawa ndi kumtumiza m'dziko lonse la colowa ca Israyeli, pakuti anacita cocititsa manyazi ndi copusa m'lsrayeli.

7 Taonani, inu nonse, ndinu ana a Israyeli, mudzinenere mau ndi kudzipangira nokha kuno.

8 Ndipo anthu onse anauka ngati munthu mmodzi, ndi kuti, Palibe mmodzi wa ife adzamuka kuhema kwace, kapena kupambukira nyumba yace,

9 koma tsopano ici ndico tidzacitira Gibeya: tidzaukwerera ndi kulota maere.

10 Ndipo tidzatapa amuna khumi limodzi pa zana limodzi, mwa mapfuko onse a Israyeli; ndi zana limodzi pa zikwi cimodzi, ndi cikwi cimodzi pa zikwi khumi kutengera anthu kamba; kuti pakufika ku Gibeya wa Benjamini, aucitire monga mwa copusa conse unacita m'Israyeli.

11 Potero amuna onse a Israyeli anasonkhanira mudziwo, olunzika ngati munthu mmodzi.

12 Ndipo mapfuko a Israyeli anatuma anthu mwa pfuko lonse la Benjamini, ndi kuti, Coipa canji ici cinacitika mwa inu?

13 Ndipo tsopano perekani amunawo otama zopanda pace, okhala m'Gibeya, kuti tiwaphe, ndi kucotsera Israyeli coipaci. Koma Benjamini sanafuna kumvera mau a abale ao, ana a Israyeli.

14 Ndipo ana a Benjamini anasonkhana kucokera ku midzi kumka ku Gibeya, kuti aturuke kulimbana ndi ana a Israyeli.

15 Ndipo anawerenga ana a Benjamini a m'midzi tsiku lija amuna zikwi makumi awiri mphambu zisanu ndi cimodzi akusolola lupanga; osawerenga okhala m'Gibeya, ndiwo amuna osankhika mazana asanu ndi awiri.

16 Mwa anthu awa onse munali amuna osankhika mazana asanu ndi awiri amanzere, yense wa iwo amaponya mwala mwa maluli osaphonya.

17 Ndipo anawerenga amuna a Israyeli, osati Benjamini, amuna zikwi mazana anai osolola lupanga, anthu a nkhondo okha okha.

18 Nauka ana a Israyeli, nakwera kumka ku Beteli, nafunsira kwa Mulungu, nati, Ayambe ndani kutikwerera pa ana a Benjamini? Ndipo Yehova anati, Ayambe ndi Yuda.

19 Nauka ana a Israyeli m'mawa, naumangira Gibeya misasa.

20 Ndipo amuna a Israyeli anaturuka kulimbana ndi Benjamini; ndi amuna a Israyeli anawandandalikira nkhondo ku Gibeya.

21 Pamenepo ana a Benjamini anaturuka m'Gibeya, naononga a Israyeli tsiku lija zikwi makumi awiri mphambu ziwiri, kuwagoneka pansi,

22 Koma anthu, ndiwo amuna a Israyeli, anadzilimbitsa nanikanso nkhondo kumene anandandalika tsiku loyambalo.

23 Ndipo ana a Israyeli anakwera nalira misozi pamaso pa Yehova mpaka madzulo; nafunsira kwa Yehova ndi kuti, Ndiyandikizenso kodi kulimbana nkhondo ndi ana a Benjamini mbale wanga? Ndipo Yehova anati, Mumkwerere.

24 Potero ana a Israyeli anayandikira ana a Benjamini m'mawa mwace.

25 Ndipo Benjamini anawaturukira ku Gibeya m'mawa mwace, naononganso a ana a Israyeli amuna zikwi khumi ndi zisanu ndi zitatu kuwagoneka pansi; ndiwo onse osolola lupanga.

26 Pamenepo ana onse a Israyeli ndi anthu onse anakwera nafika ku Beteli, nalira misozi, nakhala pansi pomwepo pamaso pa Yehova, nasala cakudya tsiku lomwelo mpaka madzulo; napereka nsembe zopsereza ndi nsembe zoyamika pamaso pa Yehova.

27 Ndipo ana a Israyeli anafunsira kwa Yehova; pakuti likasa la cipangano la Mulungu linakhala komweko masiku aja,

28 namaima ku likasalo Pinehasi mwana wa Eleazare mwana wa Aroni, masiku aja; nati, Kodi nditurukenso kulimbana nkhondo ndi ana a Benjamini mbale wanga, kapena ndileke Ndipo Yehova anati, Kwerani, pakuti mawa ndidzampereka m'dzanja lako.

29 Ndipo Israyeli anaika olalira Gibeya pozungulira pace.

30 Ndipo ana a Israyeli anakwerera ana a Benjamini tsiku lacitatu, na nika pa Gibeya monga nthawi zina.

31 Naturuka ana a Benjamini kukomana ndi anthuwo, nakokedwa kutali ndi mudzi, nayamba kuwakantha ndi kuwapha anthu amuna a Israyeli, ngati makumi atatu monga nthawi zina, m'makwalala, limodzi la awo lokwera kumka ku Beteli, ndi lina ku Gibeya kuthengo.

32 Ndipo ana a Benjamini anati, Tawakantha pamaso pathu monga poyamba paja. Koma ana a Israyeli anati, Tithawe, tiwakokere kutari ndi mudzi kumakwalala.

33 Nauka amuna onse a Israyeli m'malo ao nanika ku Baalatamari; naturuka Aisrayeli olalira aja m'malo mwao, m'Maare-geba.

34 Ndipo anadza pandunji pa Gibeya amuna osankhika m'Israyeli monse zikwi khumi, nikula nkhondo; koma sanadziwa kuti coipa ciri pafupi kuwakhudza.

35 Ndipo Yehova anakantha Benjamini pamaso pa Israyeli; ndi ana a Israyeli anawaononga a Benjamini tsiku lija amuna zikwi makumi awiri ndi zisanu, kudza zana limodzi; awa onse ndiwo akusolola lupanga.

36 Ndipo ana a Benjamini anaona kuti takanthidwa; popeza amuna a Israyeli anawapatsa Abenjamini malo, pakuti anatama olalira amene anawaikiratu pa Gibeya.

37 Nafulumira olalirawo nathamangira Gibeya, nabalalika olalirawo, nakantha mudzi wonse ndi lupanga lakuthwa.

38 Koma kunali cizindikilo coikika pakati pa amuna a Israyeli ndi olalirawo, ndico cakuti afukitse mtambo wa utsi kumudzi.

39 Ndi nkhondo ya Israyeli inathawa, ndipo Benjamini anayamba kuwakantha ndi kuwagwaza amuna a Israyeli, ngati amuna makumi atatu, pakuti anati, Ndithu Tawakantha konse pamaso pathu, monga ku nkhondo yoyambayo.

40 Koma pamene mtambo unayamba kukwera m'mudzi ngati utsi uti tolo, Abenjamini anaceuka, ndipo taonani, pamodzi ponse panafuka utsi kumwamba.

41 Natembenuka amuna a Israyeli; nadabwa amuna a Benjamini; popeza anaona kuti cidawagwera coipa.

42 Nabwerera iwo pamaso pa amuna a Israyeli kumka njira ya cipululu; koma nkhondo inawaloodetsa; ndi aja oturuka m'mudzi anawaononga pakati pao.

43 Anawazinga Abenjamini, anawapitikitsa, nawapondereza pampumulo mpaka pandunji pa Gibeya, koturukira dzuwa.

44 Ndipo adagwa a Benjamini amuna zikwi khumi ndi zisanu ndi zitatu; iwo onse ndiwo ngwazi.

45 Natembenuka iwo, nathawira kucipululu ku thanthwe la Rimoni; koma anawakunkha m'makwalala amuna zikwi zisanu; nawalondetsa ku Gidomu, nakantha a iwowa amuna zikwi ziwiri.

46 Potero onse amene adagwa a Benjamini tsiku lija, ndiwo amuna zikwi makumi awiri mphambu zisanu, akusolola lupanga; iwo onse ndiwo ngwazi.

47 Koma amuna mazana asanu ndi limodzi anabwerera nathawira kucipululu, ku thanthwe la Rimoni, nakhala m'thanthwe la Rimoni miyezi inai.

48 Ndipo amuna a Israyeli anabwereranso kwa ana a Benjamini, nawakantha ndi lupanga lakuthwa a m'mudzi wonse, ndi zoweta, ndi zonse adazipeza; anatenthanso midzi yonse anaipeza.

21

1 Koma amuna a Israyeli adalumbira ku Mizipa, ndi kuti, Palibe mmodzi wa ife adzapereka mwana wace wamkazi kwa Mbenjamini akhale mkazi wace.

2 Ndipo anthu anadza ku Beteli, nakhala pansi pomwepo pamaso pa Mulungu mpaka madzulo; nakweza mau ao ndi kulira misozi yambiri.

3 Nati iwo, Yehova Mulungu wa Israyeli, cacitika ici cifukwa ninji m'Israyeli kuti lasowa lero pfuko limodzi m'Israyeli?

4 Ndipo kunali m'mawa mwace, anthu analawirira mamawa namangako guwa la nsembe, napereka nsembe zopsereza ndi nsembe zoyamika.

5 Nati ana a Israyeli, Ndani iye mwa mapfuko onse a Israyeli amene sanakwera kudza kumsonkhano kwa Yehova? pakuti panali lumbiro lalikuru pa iye wosakwera kudza kwa Yehova ku Mizipa, ndi kuti, Aphedwe ndithu.

6 Ndipo ana a Israyeli anamva cifundo cifukwa ca Benjamini mbale wao, nati, Pfuko limodzi lalikhidwa pa Israyeli leroli.

7 Tidzatani kuwafunira otsalawo akazi, popeza tinalumbira ife pa Yehova kuti sitidzawapatsa ana athu akazi akhale akazi ao?

8 Nati iwo, Kodi pali lina la mapfuko a Israyeli losakwera kudza kwa Yehova ku Mizipa? Ndipo taonani, kucokera ku Yabesi-gileadi sanadza mmodzi kumisasa, kumsonkhano.

9 Pakuti pamene anawerenga anthu, taonani, panalibe mmodzi komweko wa okhala m'Yabesi-gileadi,

10 Ndipo msonkhano unatumizako amuna zikwi khumi ndi ziwiri, ndiwo ngwazi, nawalamulira ndi kuti, Mukani, nimuwakanthe okhala m'Yabesi-gileadi ndi lupanga lakuthwa, ndi akazi ndi ana ang'ono.

11 Ndipo cimene mukacite ndi ici: mukaononge konse mwamuna ali yense, ndi mkazi ali yense wodziwa mwamuna mogona naye.

12 Ndipo anapeza mwa anthu a Yabesi-gileadi anamwali mazana anai osadziwa mwamuna mogona naye; nabwera nao kumisasa ku Silo, ndiwo a m'dziko la Kanani.

13 Ndipo msonkhano wonse unatumiza mau kwa ana a Benjamini okhala m'thanthwe la Rimoni, nawalalikira mtendere.

14 Nakwera Abenjamini nthawi ija, ndipo anawapatsa akazi amene anawasunga amoyo mwa akazi a Yabesi-gileadi; koma sanawafikira.

15 Ndipo anthu anamva cifundo pa Benjamini, pakuti Yehova adang'amba mapfuko a Israyeli.

16 Pamenepo akuru a msonkhano anati, Tidzatani, kuwafunira akazi otsalawo, popeza akazi anatha psiti m'Benjamini?

17 Nati iwo, Pakhale colowa ca iwo opulumuka a Benjamini, lingafafanizidwe pfuko m'Israyeli.

18 Koma sitikhoza ife kuwapatsa ana athu akazi akhale akazi ao; pakuti ana a Israyeli adalumbira ndi kuti, Atembereredwe wakupatsa Abenjamini mkazi.

19 Natiiwo, Taonani, pali madyerero a Yehova caka ndi caka ku Silo, ndiko kumpoto kwa Beteli, kum'mawa kwa mseu wokwera kucokera ku Beteli kumka ku Sekemu, ndi kumwela kwa Lebona.

20 Ndipo analamulira ana a Benjamini ndi kuti, Mukani, mulalire m'minda yamphesa;

21 nimuyang'ane, ndipo taonani, ataturuka ana akazi a Silo kubvinabvina, pamenepo muturuke m'minda yamphesa ndi kudzigwirira yense mkazi wace mwa ana akazi a Silo, ndi kumuka naye ku dziko la Benjamini.

22 Ndipo kudzali, akatifikira atate ao kapena alongo ao kunena nafe mlandu, tidzanena nao, Mutipatse awa, pakuti sitinawatengera yense mkazi wace kunkhondo; pakuti inunso simunawaninkha awa; mukadatero mukadaparamula tsopano.

23 Nacita cotere ana a Benjamini, nadzitengera akazi monga mwa kuwerenga kwao, a obvina aja, amene anawatenga mwacifwamba; namuka iwo nabwerera ku colowa cao, namanga midzi, nakhalamo.

24 Ndipo ana a Israyeli anacokako nthawi ija yense kumka ku pfuko lace, ndi banja lace, naturukako yense kumka ku colowa cace.

25 Panalibe mfumu m'Israyeli masiku aja; a yense anacita comkomera pamaso pace.