1 NDIPO mfumu Davide anakalamba nacuruka masiku ace; ndipo iwo anampfunda ndi zopfunda, koma iye sanafundidwa.
2 Pamenepo anyamata ace ananena naye, Amfunire mbuye wanga mfumu namwali, aimirire pamaso pa mfumu namsunge; nagone m'mfukato mwanu, kuti mbuye mfumu yanga afundidwe.
3 Tsono anafunafuna m'malire monse a Israyeli namwali wokongola, napeza Abisagi wa ku-Sunamu, nabwera naye kwa mfumu.
4 Ndipo namwaliyo anali wokongola ndithu, namasunga mfumu namtumikira; koma mfumu sinamdziwa.
5 Pamenepo Adoniya mwana wa Hagiti anadzikuza, nati, Ndikhala mfumu ndine; nadzikonzera agareta ndi apakavalo ndi anthu makumi asanu omtsogolera mothamanga.
6 Ndipo atate wace sadambvuta masiku ace onse, ndi kuti, Wlitero cifukwa ninji? Ndiponso anali munthu wokongola ndithu; napondana ndi Abisalomu.
7 Ndipo anapangana ndi Yoabu mwana wa Zeruya, ndi Abyatara wansembeyo; ndipo amenewo anamtsata Adoniya namthandiza.
8 Koma Zadoki wansembe, ndi Benaya mwana wace wa Yehoyada, ndi Natani mneneri, ndi Simeyi, ndi Reyi, ndi anthu amphamvu aja adali ndi Davide, sanali ndi Adoniya.
9 Ndipo Adoniya anapha nkhosa ndi ng'ombe ndi nyama zonona pamwala pa Zoheleti, uli pafupi ndi citsime ca Rogeli, naitana abale ace onse ana a mfumu, ndi anthu onse a Yuda anayamata a mfumu;
10 koma Natani mneneriyo, ndi Benaya, ndi anthu amphamvu aja, ndi Solomo mbale wace, sanawaitana.
11 Pamenepo Natani ananena ndi Batiseba amace wa Solomo, nati, Kodi sunamva kuti Adoniya mwana wa Hagiti walowa ufumu, ndipo Davide mbuye wathu sadziwa?
12 Ubwere tsono, ndikupangire, kuti usunge moyo wako, ndi moyo wa mwana wako Solomo.
13 Muka nulowe kwa mfumu Davide, nukati kwa iye, Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbirira mdzakazi wanu, ndi kuti, Zedi Solomo mwana wako adzakhala mfumu nditamuka ine, nadzakhala pa mpando wanga wadfumu? ndipo Adoniya akhaliranji mfumu?
14 Taona, uli cilankhulire ndi mfumu, inenso ndidzalowa pambuyo pako, ndi kutsimikiza mau ako.
15 Pamenepo Batiseba analowa kwa mfumu kucipinda; ndipo mfumuyo inali yokalamba ndithu; ndipo Abisagi wa ku Sunamu anali kutumikira mfumu.
16 Ndipo Batiseba anawerama nalambira mfumu, ndi mfumu niti, Ufunanji?
17 Ndipo iye ananena nayo, Mbuye wanga, munalumbirira mdzakazi wanu pa Yehova Mulungu wanu, ndi kuti, Zedi Solomo mwana wako adzakhala mfumu nditamuka ine, nadzakhala pa mpando wanga wacifumu.
18 Ndipo tsopano taonani, Adoniva walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu simudziwa.
19 Ndipo iye anapha ng'ombe ndi nyama zonona ndi nkhosa zaunyinji, naitana ana amuna onse a mfumu, ndi Abyatara wansembe, ndi Yoabu kazembe wa nkhondo; koma Solomo mnyamata wanu sanamuitana.
20 Ndipo tsopano, mbuye wanga mfumu, maso a Aisrayeli onse ali pa inu, kuti muwauze amene adzakhala pa mpando wacifumu wa mbuye wanga mfumu atamuka iye,
21 Mukapanda kutero, kudzacitika, pamene mbuye wanga mfumu atagona kwa makolo ace, ine ndi mwana wanga Solomo tidzayesedwa ocimwa.
22 Ndipo taona, iye ali cilankhulire ndi mfumu, Natani mneneriyo analowamo.
23 Ndipo anauza mfumu, kuti, Wafika Natani mneneriyo. Ndipo iye anafika pamaso pa mfumu, naweramitsa nkhope yace pansi pamaso pa mfumu.
24 Ndipo Natani anati, Mbuye wanga mfumu, kodi inu munati, Adoniya adzakhala mfumu nditamuka ine, nadzakhala ndiye pa mpando wanga wacifumu?
25 Popeza iye watsika lero, nakapha ng'ombe ndi nyama zonona ndi nkhosa zaunyinji, naitana ana amuna onse a mfumu, ndi akazembe a nkhondo, ndi Abyatara wansembe; ndipo taonani, iwowo akudya ndi kumwa pamaso pace, nati, Akhale ndi moyo mfumu Adoniya.
26 Koma ine, inde inedi mnyamata wanu, ndi Zadoki wansembe, ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndi Solomo mnyamata wanu, sanatiitana.
27 Cinthu ici cacitika ndi mbuye wanga mfumu kodi, ndipo simunadziwitsa mnyamata wanu amene adzakhala pa mpando wacifumu wa mbuye wanga mfumu atamuka iye?
28 Tsono mfumu Davide anayankha, nati, Ndiitanireni Batiseba. Ndipo iye analowa pamaso pa mfumu, naima pamaso pa mfumu.
29 Ndipo mfumu inalumbira, niti, Pali Yehova amene anapulumutsa moyo wanga m'nsautso monse,
30 zedi monga umo ndinalumbirira iwe pa Yehova Mulungu wa Israyeli, ndi kuti, Zoonadi Solomo mwana wako adzakhala mfumu nditamuka ine, nadzakhala pa mpando wanga wacifumu m'malo mwa ine, zedi nditero lero lomwe.
31 Pamenepo Batiseba anaweramitsa pansi nkhope yace, nalambira mfumu, nati, Mbuye wanga mfumuakhale ndi moyo nthawi zamuyaya.
32 Ndipo mfumu Davide anati, Kandiitanireni Zadoki wansembeyo, ndi Natani mneneriyo, ndi Benaya mwana wa Yehoyada. Iwo nalowa pamaso pa mfumu.
33 Ndipo mfumu inati kwa iwo, Tengani akapolo a mfumu yanu, nimukweze Solomo mwana wanga pa nyuru yanga yanga, nimutsikire naye ku Gihoni.
34 Ndipo Zadoki wansembe ndi Natani mneneri akamdzoze kumeneko akhale mfumu ya Israyeli; ndipo muombe lipenga, ndi kuti, Mfumu Solomo akhale ndi moyo.
35 Pamenepo mumtsate iye, iye nadzadza nadzakhala pa mpando wanga wacifumu, popeza adzakhala iyeyu mfumu m'malo mwanga; ndipo ndamuika iye akhale mtsogoleri wa lsrayeli ndi Yuda.
36 Ndipo Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu, nati, Amen, ateronso Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu.
37 Monga umo Yehova anakhalira ndi mbuye wanga mfumu, momwemo akhalenso ndi Solomo, nakuze mpando wace wacifumu upose mpando wacifumu wa mbuye wanga mfumu Davide.
38 Pamenepo Zadoki wansembe, ndi Natani mneneri, ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndi Akereti, ndi Apeleti aja anatsika, nakweza Solomo pa nyuru ya mfumu Davide, nafika naye ku Gihoni.
39 Ndipo Zadoki wansembe anatenga nyanga ya mafuta inali m'Cihema, namdzoza Solomo. Ndipo iwo anaomba lipenga, ndi anthu onse anati, Mfumu Solomo akhale ndi moyo.
40 Ndipo anthu onse anakwera namtsata, naliza zitoliro, nakondwera ndi kukondwera kwakukuru, kotero kuti pansi panang'ambikandiphokosolao.
41 Ndipo Adoniya ndi oitanidwa onse anali ndi iye analimva atatha kudya. Ndipo Yoabu, pakumva kuomba kwa lipengalo, anati, Phokosolo ndi ciani kuti m'mudzi muli cibumo?
42 iye akali cilankhulire, taona, walowa Yonatani mwana wa Abyatara wansembe, ndipo Adoniya anati, Lowa, popeza ndiwe munthu wamphamvu, nubwera nao uthenga wabwino.
43 Ndipo Yonatani anayankha, nati kwa Adoniya, Zedi Davide mbuye wathu mfumu walonga Solomo ufumu:
44 ndipo mfumu yatumanso Zadoki wansembe, ndi Natani mneneri, ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndi Akereti, ndi Apeleti aja, namkweza iye pa nyuru ya mfumu.
45 Ndipo Zadoki wansembe ndi Natani mneneri anamdzoza mfumu ku Gihoni, ndipo acokera kwneneko cikondwerere, ndi m'mudzimo muli phokoso. Ndilo phokoso limene mwamvali.
46 Ndiponso Solomo wakhala pa cimpando ca ufumu.
47 Ndiponso akapolo a mfumu anadzadalitsa Davide mbuye wathu mfumu, nati, Mulungu wanu aposetse dzina la Solomo lipunde dzina lanu, nakulitse mpando wace wacifumu upose mpando wanu wacifumu; ndipo mfumu anawerama pakamapo.
48 Ndiponso watero mfumu, Wolemekezeka Yehova Mulungu wa Israyeli, amene wapereka lero wina wokhala pa mpando wanga wacifumu, maso anga ali cipenyere.
49 Pamenepo oitanidwa onse a Adoniya anacita mantha, nanyamuka, napita yense njira yace.
50 Ndipo Adoniya anaopa cifukwa ca Solomo, nanyamuka, nakagwira nyanga za guwa la nsembe.
51 Ndipo anthu anakauza Solomo, kuti, Taonani, Adoniya aopa mfumu Solomo, popeza taonani, wagwira nyanga za guwa la nsembe, nati, Mfumu Solomo alumbirire ine lero kuti sadzandipha kapolo wace ndi lupanga.
52 Ndipo Solomo anati, iye akakhala munthu woyenera silidzagwa pansi tsitsi lace limodzi lonse; koma mukapezeka mwa iye coipa, adzafadi.
53 Tsono mfumu Solomo anatuma anthu nakamtsitsa ku guwa la nsembe. Iye nadza, nagwadira mfumu Solomo; Solomo nati kwa iye, Pita kwanu.
1 Pakuyandikira masiku ace a Davide akuti amwalire, analamulira Solomo mwana wace, nati,
2 Ndimuka ine njira ya dziko lonse: limba mtima tsono, nudzionetse umunthu;
3 nusunge cilangizo ca Yehova Mulungu wako, kuyenda m'njira zace, kusunga malemba ndi malamulo ndi maweruzo ndi umboni wace, monga mulembedwa m'cilamulo ca Mose, kuti ukacite mwa nzeru m'zonse ukacitazo, ndi kumene konse ukatembenukirako;
4 kuti Yehova akakhazikitse mau ace adanenawo za ine, kuti, Ngati ana ako akasunga bwino njira zao, kuyenda moona pamaso pa Ine ndi mtima wao wonse ndi moyo wao wonse, nditi sipadzakusowa mwamuna mmodzi pa mpando wacifumu wa Israyeli.
5 Ndiponso udziwa cimene Yoabu mwana wa Zeruya anandicitira, inde cimene anawacitira akazembe awiri aja a magulu a nkhondo a Israyeli, ndiwo Abineri mwana wa Neri, ndi Amasa mwana wa Yeteri, amene aja anawapha, nakhetsa mwazi ngati wa nkhondo masiku a mtendere, napaka mwazi wa nkhondo pa lamba lace la m'cuuno mwace, ndi pa nsapato za pa mapazi ace.
6 Cita mwa nzeru yako tsono, osalola mutu wace waimvi utsikire kumanda ndi mtendere.
7 Koma ucitire zokoma ana amuna aja a Barizilai wa ku Gileadi, akhale pakati pa akudyera pa gome lako, popeza momwemo amenewo anandiyandikira muja ndinalikuthawa Abisalomu mbale wako.
8 Ndipo taona uli naye Simeyi mwana wa Gera wa pfuko la Benjamini wa ku Bahurimu, yemwe uja adanditemberera ndi temberero lalikuru tsiku lija lakupita ine ku Mahanaimu; koma anadzakomana ndi ine pa Yordano, ndipo ndinalumbirira iye pa Yehova, kuti, Sindikupha iwe ndi lupanga,
9 Ndipo tsono, usamuyesera iye wosacimwa, popeza ndiwe munthu wanzeru, ndipo udziwa umo uyenera kumcitira iye, nutsitsire mutu wace waimvi ndi mwazi kumanda.
10 Ndipo Davide anagona pamodzi ndi makolo ace, naikidwa m'mudzi wa Davide.
11 Ndipo masiku ace akukhala Davide mfumu ya Israyeli anali zaka makumi anai; zaka zisanu ndi ziwiri anakhala mfumu ku Hebroni, ndi zaka makumi atatu mphambu citatu anakhala mfumu ku Yerusalemu.
12 Tsono Solomo anakhala pa mpando wacifumu wa Davide atate wace, ndipo ufumu wace unakhazikika kwakukuru.
13 Pomwepo Adoniya mwana wa Hagati anadza kwa Batiseba amai wace wa Solomo, ndipo mkaziyo anati, Kodi wadza ndi mtendere? Nati, Ndi mtendere umene.
14 Anatinso, Ndiri nanu mau, Nati iye, Tanena.
15 Nati iye, Mudziwa kuti ufumu unali wanga, ndi kuti Aisrayeli onse anaika maso ao pa ine, kuti ndikhale mfumu ndine; koma ufumu watembenuka nukhala wa mbale wanga, popeza iye anaulandira kwa Mulungu.
16 Ndipo tsopano, ndikupemphani pempho limodzi, musandikaniza. Ndipo mkaziyo anati kwa iye, Tanena.
17 Nati iye, Mundinenere kwa mfumu Solomo, popeza sakukanizani, kuti andipatse Abisagi wa ku Sunamu akhale mkazi wanga.
18 Ndipo Batiseba anati, Cabwino, ndidzakunenera kwa mfumu.
19 Tsono Batiseba ananka kwa mfumu Solomo kukanenera Adoniya kwa iye. Ndipo mfumu inanyamuka kukomana naye, namuweramira nakhalanso pa mpando wace wacifumu, naikitsa mpando wina wa amace wa mfumu, nakhala iye ku dzanja lace lamanja.
20 Pamenepo mkaziyo anati, Ndikupemphani kapempho kamodzi, musandikaniza. Ndipo mfumu inati kwa iye, Tapemphani amai wanga, popeza sindikukanizani.
21 Ndipo iye anati, Abisagi wa ku Sunamu apatsidwe kwa Adoniya mbale wanu akhale mkazi wace.
22 Ndipo mfumu Solomo anayankha, nati kwa amai wace, Mupempheranji Abisagi wa ku Sunamu akhale wace wa Adoniya? Mumpempherenso ufumu, popeza ndiye mkuru wanga; inde ukhale wace, ndi wa Abyatara wansembeyo, ndi wa Yoabu mwana wa Zeruya.
23 Pomwepo mfumu Solomo analumbira pa Yehova, nati, Mulungu andilange naonjezepo, zedi Adoniya wadziphetsa yekha ndi mau awa.
24 Ndipo tsono, pali Yehova amene wandikhazikitsa ine, nandikhalitsa pampando wacifumu wa Davide atate wanga, nandimangira nyumba monga analonjeza, zedi Adoniya aphedwa lero lomwe.
25 Ndipo mfumu Solomo anatuma dzanja la Benaya mwana wa Yehoyada, ndipo anamgwera, namwalira iye.
26 Ndipo mfumu inanena ndi Abyatara wansembeyo, Pita ku Anatoti ku minda yako; pakuti wakutidwa ndi imfa; koma sindikupha iwe lero lino, cifukwa unanyamula likasa la Ambuye Yehova pamaso pa Davide atate wanga, ndi popeza unazunzidwa monse umo atate wanga Davide anazunzidwamo.
27 Motero Solomo anacotsa Abyatara asakhalenso wansembe wa Yehova, kuti akakwaniritse mau a Yehova amene aja adalankhula ku Silo za mbumba ya Eli.
28 Ndipo mbiriyi inamfika Yoabu, pakuti Yoabu anapambukira kwa Adoniya, angakhale sanapambukira kwa Abisalomu. Ndipo Yoabu anathawira ku cihema ca Yehova, nagwira nyanga za guwa la nsembe.
29 Ndipo anamuuza mfumu Solomo, kuti, Yoabu wathawira ku cihema ca Yehova; ndipo taonani, wakhala ku guwa la nsembe. Pomwepo Solomo anatuma Benaya mwana wa Yehoyada, nati, Kamkwereo
30 Nafika Benaya ku cihema ca Yehova, nati kwa iye, Mfumu itero, Taturuka. Nati, Iai, koma ndifere pompano. Ndipo Benaya anabweza mau kwa mfumu, nati, Yoabu wanena cakuti, nandiyankha mwakuti mwakuti.
31 Ndipo mfumu inati kwa iye, Cita monga umo wanena iye, numkwere, numuike; kuti undicotsere ine ndi nyumba ya atate wanga mwazi uja Yoabu anaukhetsa wopanda cifukwa.
32 Ndipo Yehova adzambwezera mwazi wace pa mutu wace wa iye yekha, popeza iye anawakantha anthu awiri olungama ndi okoma oposa iye mwini, nawapha ndi lupanga, atate wanga Davide osadziwa, ndiwo Abineri mwana wa Neri kazembe wa khamu la nkhondo la Israyeli, ndi Amasa mwana wa Yeteri kazembe wa khamu la nkhondo la Yuda.
33 Motero mwazi wao udzabweranso pa mutu wace wa Yoabu, ndi pa mutu wa mbumba yace, ku nthawi yamuyaya; koma Davide, ndi mbumba yace, ndi banja lace, ndi mpando wace wacifumu adzakhala ndi mtendere wa Yehova ku nthawi yamuyaya.
34 Pomwepo Benaya mwana wa Yehoyada anakwera namkantha iye, namupha; ndipo anaikidwa m'nyumba yace yace kucipululu.
35 Ndipo mfumu inaika Benaya mwana wa Yehoyada m'malo mwace kutsogolera khamu la nkhondo, ndi mfumu inaika Zadoki wansembe m'malo mwa Abyatara.
36 Ndipo mfumu inatuma munthu kukaitana Simeyi, nati kwa iye, Udzimangire nyumba m'Yerusalemu, nukhale komweko osaturukako kumka kwina konse.
37 Popeza tsiku lomwelo lakuturuka iwe ndi kuoloka mtsinje Kidroni, tadziwa ndithu kuti udzafadi, mwazi wako udzakhala pa mutu wa iwe wekha.
38 Ndipo Simeyi ananena ndi mfumu, Mau awa ndi abwino; monga momwe mwanena mbuye wanga mfumu momwemo ndidzacita kapolo wanu. Ndipo Simeyi anakhala m'Yerusalemu masiku ambiri.
39 Ndipo kunacitika, zitapita zaka zitatu, kuti akapolo awiri a Simeyi anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka mfumu ya Gati. Ndipo anamuuza Simeyi, nati, Taonani, akapolo anu akhala ku Gati.
40 Ndipo Simeyi ananyamuka, namangirira mbereko pa buru wace, namka ku Gati kwa Akisi kukafuna aka polo ace; namuka Simeyi, nabwera nao akapolo ace kucokera ku Gati.
41 Ndipo anamuuza Solomo, kuti, Simeyi wacoka ku Yerusalemu kumka ku Gati, nabweranso.
42 Ndipo mfumu inatuma munthu kukaitana Simeyi, niti kwa iye, Kodi sindinakulumbiritsa pa Yehova ndi kukucenjeza, kuti, Tadziwa ndithu, kuti tsiku lakuturuka iwe ndi kukayenda kwina konse udzafa ndithu? Ndipo iwe unati kwa ine, Mau amene ndawamva ndi abwino.
43 Sunasunga cifukwa ninji lumbiro la pa Yehova, ndi lamulo lija ndinakulamulira iwe?
44 Tsono mfumu inanenanso ndi Simeyi, Udziwa iwe coipa conse mtima wako umadziwaco, cimene udacitira Davide atate wanga; cifukwa cace Yehova adzakubwezera coipa cako pamutu pako mwini.
45 Koma mfumu Solomo adzadalitsika, ndi mpando wacifumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova ku nthawi yamuyaya.
46 Pamenepo mfumu inalamulira Benaya mwana wa Yehoyada, ndipo iye anaturuka namkwera, namwalira iye. Ndipo ufumu unakhazikika m'dzanja la Solomo.
1 Ndipo Solomo anapalana ubwenzi ndi Farao mfumu ya Aigupto, natenga mwana wamkazi wa Farao, nadza naye ku mudzi wa Davide, mpaka atamanga nyumba ya iye yekha, ndi nyumba ya Yehova, ndi linga lozinga Yerusalemu.
2 Koma anthu anaphera nsembe pamisanje, popeza panalibe nyumba yomangira dzina la Yehova kufikira masiku omwewo.
3 Ndipo Solomo anakondana ndi Yehova, nayenda m'malemba a Davide atate wace; koma anaphera nsembe nafukiza zonunkhira pamisanje.
4 Ndipo mfumu inapita ku Gibeoni kukaphera nsembe kumeneko; popeza msanje waukuru unali kumeneko, Solomo anapereka nsembe zopsereza cikwi cimodzi pa guwalo la nsembe.
5 Ku Gibeoni Yehova anaonekera Solomo m'kulota usiku, nati Mulungu, Tapempha cimene ndikupatse.
6 Ndipo Solomo anati, Munamcitira mtumiki wanu Davide atate wanga zokoma zazikulu, monga umo anayenda pamaso panu ndi coonadi ndi cilungamo ndi mtima woongoka ndi Inu; ndipo mwamsungira cokoma ici cacikuru kuti mwampatsa mwana kukhala pa mpando wace wacifumu monga lero lino.
7 Ndipo tsopano, Yehova Inu Mulungu wanga, mwalonga ine kapolo wanu ufumu m'malo mwa atate wanga Davide, koma ine ndine kamwana, sindidziwa kuturuka kapena kulowa.
8 Ndipo kapolo wanu ndiri pakati pa anthu anu amene Inu munawasankha, anthu ambirimbiri osawerengeka, kapena kulembeka m'unyinji wao.
9 Patsani tsono kapolo wanu mtima womvera wakuweruza anthu anu; kuti ndizindikire pakati pa zabwino ndi zoipa; pakuti akutha ndani kuweruza anthu anu ambiri amene?
10 Ndipo mau amenewa anakondweretsa Yehova kuti Solomo anapempha cimeneci.
11 Ndipo Mulungu anati kwa iye, Popeza wapempha cimeneci, osadzipemphera masiku ambiri, osadzipempheranso cuma, osadzipempheranso moyo wa adani ako, koma wadzipemphera nzeru zakumvera mirandu;
12 taona, ndacita monga mwa mau ako; taona ndakupatsa mtima wanzeru ndi wakuzindikira, kotero kuti panalibe wina wolingana ndi iwe kale, ndipo sadzakhalanso wina wolingana ndi iwe utamuka.
13 Ndiponso zimene sunazipempha adakupatsa, ndipo cuma ndi ulemu, kuti pakati pa mafumu sipadzakhala yina yolingana ndi iwe masiku ako onse.
14 Ndipo ukadzayenda m'njira zanga kusunga malemba anga ndi malamulo anga, monga atate wako Davide anayendamo, Ine ndidzacurukitsa masiku ako.
15 Ndipo Solomo anauka, ndipo taona, ndilo loto; nabwera ku Yerusalemu, naima ku likasa la cipangano ca Yehova, napereka nsembe zopsereza ndi nsembe zamtendere, nakonzera anyamata ace onse madyerero.
16 Pamenepo analowa kwa mfumu akazi awiri, ndiwo adama, naima pamaso pace.
17 Ndipo mkazi mmodzi anati, Mbuye wanga, ine ndi mkazi uyu tikhala awiri m'nyumba imodzi; ndipo ine ndinaona mwana, iye ali m'nyumbamo.
18 Ndipo kunacitika kuti tsiku lacitatu nditaona ine mwana, mnzangayu anaonanso mwana; ndipo ife tinali pamodzi, munalibe mlendo ndi ife m'nyumbamo, koma ife awiri m'nyumbamo.
19 Ndipo mwana wa mnzangayu anamwalira usiku, pokhala iyeyu anamgonera.
20 Ndipo iye anauka pakati pa usiku, natenga mwana wanga kumimba kwanga, mdzakazi wanu ndiri m'tulo, namuika m'mfukato mwace, naika mwana wace wakufa m'mfukato mwanga.
21 Ndipo pouka ine m'mawa kuyamwitsa mwana wanga ndaona ngwakufa, koma nditamzindikira m'mawa ndaona si mwana wanga wobala ine ai.
22 Ndipo mkazi winayo anati, lai, koma wamoyoyu ndi mwana wanga, ndi wakufayu ndi mwana wako. Ndipo uja anati, lai, koma wakufayu ndi mwana wako, ndi wamoyoyu ndi mwana wanga. Motero iwo analankhula pamaso pa mfumu.
23 Tsono mfumu inati, Uyu akuti, Wamoyoyu ndiye mwana wanga ndi wakufayu ndiye mwana wako; ndipo winayo akuti, lai, koma mwana wako ndiye wakufayu, ndi mwana wanga ndiye wamoyoyu.
24 Niti mfumu, Kanaitengereni cimpeni. Ndipo iwo anabwera ndi cimpeni kwa mfumu.
25 Mfumu niti, Dula pakati mwana wamoyoyu, nupatse mmodzi cipinjiri, ndi wina cipinjiri cace.
26 Koma mkazi amene mwana wamoyo anali wace analankhula ndi mfumu, popeza mtima wace unalira mwana wace, nati, Ha! mbuye wanga, mumpatse uyo mwana wamoyo osamupha konse. Koma winayo anati, Asakhale wanga kapena wako, dulani.
27 Pamenepo mfumu inayankha, niti, Mumpatse wacifundoyo mwana wamoyo, osamupha konse, uyo ndiye amace.
28 Ndipo Aisrayeli onse anamva maweruzidwe ace idaweruza mfumu, naopa mfumu; pokhala anaona kuti nzeru ya Mulungu inali mwa iye yakuweruza.
1 Ndipo mfumu Solomo anali mfumu ya Israyeli yense.
2 Ndipo akuru a mfumu ndi awa: Azariya mwana wa Zadoki anali nduna,
3 Elihorepa ndi Ahiya ana a Sisa alembi, Yehosafati mwana wa Ahiludi wolembera mbiri,
4 ndi Benaya mwana wa Yehoyada anali kazembe wa nkhondo, ndi Zadoki ndi Abyatara anali ansembe,
5 ndi Azariya mwana wa Natani anayang'anira akapitao, ndi Zabudi mwana wa Natani anali nduna yopangira mfumu,
6 ndi Ahisara anayang'anira banja la mfumu, ndi Adoniramu mwana wa Abida anali wamsonkho.
7 Ndipo Solomo anali nao akapitao khumi ndi awiri akuyang'anira Aisrayeli onse, akufikitsira mfumu ndi banja lace zakudya; ali yense anafikitsa zakudya zofikira mwezi umodzi wa caka.
8 Ndipo maina ao ndiwo: Benhuri anatengetsa ku mapiri a Efraimu;
9 Bendekeri ku Makazi ndi Saalibimu ndi Betsemesi ndi Elonibetanani;
10 Benhesedi ku Aruboti ndi Soko ndi dziko lonse la Heferi;
11 Benabinadabu ku mtunda wa Dori, mkazi wace ndiye Tafati mwana wa Solomo;
12 Baana mwana wa Ahiludi ku Tanaki ndi Megido ndi Betseani konse, ali pafupi ndi Zaratana kunsi kwa Yezreeli, kuyambira ku Betseani kufikira ku Abelimehola, kufikiranso kundunji ku Yokineamu;
13 Benigeheri ku Ramoti Gileadi, iyeyo anali nayo midzi ya Yairo mwana wa Manase iri m'Gileadiyo, iye anali nalo dziko la Arigobi liri m'Basani, midzi yaikuru makumi asanu ndi limodzi yamalinga ndi zitseko zamkuwa;
14 Abinadabu mwana wa Ido ku Nahanaimu;
15 Ahimazi ku Nafitali, iyeyu adakwatira Basemati mwana wa Solomo;
16 Baana mwana wa Husayi ku Aseri ndi ku Aloti;
17 Yehosafati mwana wa Paruwa ku Isakara;
18 Simeyi mwana wa Ela ku Benjamini;
19 Geberi mwana wa Uri ku dziko la Gileadi, dziko la Sihoni mfumu ya Aamori, ndi la Ogi mfumu ya Basani; munalibe kapitao wina m'deramo.
20 Ayuda ndi Aisrayeli anacuruka ngati mcenga wa kunyanja, namadya namamwa namakondwera.
21 Ndipo Solomo analamulira maiko onse, kuyambira ku Firate kufikira ku dziko la Afilisti ndi ku malire a Aigupto; anthu anabwera nayo mitulo namtumikira Solomo masiku onse a moyo wace.
22 Ndipo zakudya za Solomo zofikira tsiku limodzi zinalr miyeso makumi atatu ya ufa wosalala, ndi miyeso makumi asanu ndi limodzi ya ufa wamankhupete,
23 ng'ombe zonenepa khumi, ndi ng'ombe za kubusa makumi awiri, ndi nkhosa zana limodzi, osawerenganso ngondo ndi nswala ndi mphoyo ndi mbalame zoweta.
24 Pakuti analamulira dziko lonse liri tsidya lino la Firate, kuyambira ku Tipsa kufikira ku Gaza, inde mafumu onse a ku tsidya tino la Firate; nakhala ndi mtendere kozungulira konseko,
25 Ndipo Ayuda ndi Aisrayeli anakhala mosatekeseka, munthu yense patsinde pa mpesa wace ndi mkuyu wace, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba, masiku onse a Solomo.
26 Ndipo Solomo anali nazo zipinda za akavalo a magareta ace zikwi makumi anai, ndi apakavalo zikwi khumi mphambu ziwiri.
27 Ndipo akapitao aja anatengetsera cakudya Solomo ndi anthu onse akudya ku gome la mfumu Solomo, munthu yense m'mwezi mwace, sanalola kanthu kasoweke.
28 Barelenso ndi udzu wa akavalo ndi ngamila anabwera nazo kumalo kwao, munthu yense monga momwe anamuuzira.
29 Ndipo Mulungu anampatsa Solomo nzeru ndi luntha lambiri, ndi mtima wodziwa za mitundu mitundu, zonga mcenga uli m'mbali mwa nyanja.
30 Ndipo nzeru ya Solomo inaposa nzeru za anthu onse a kum'mawa, ndi nzeru zonse za ku Aigupto.
31 Pakuti anali wanzeru woposa anthu onse, woposa Etani wa ku Ezra, ndi Hemani, ndi Kalikoli, ndi Darida ana a Maholi; ndipo mbiri yace inafikira amitundu onse ozungulira.
32 Ndipo ananena miyambo zikwi zitatu, ndipo nyimbo zace zinali cikwi cimodzi mphambu zisanu.
33 Nakamba za mitengo, kuyambira mkungudza uli ku Lebano kufikira hisopi wophuka pakhoma; anakambanso za nyama ndi mbalame ndi zinthu zokwawa pansi ndi za nsomba.
34 Ndipo anafikako anthu a mitundu yonse kudzamva nzeru ya Solomo, ocokera kwa mafumu onse a dziko lonse lapansi, amene adamva mbiri ya nzeru yace.
1 Ndipo Hiramu mfumu ya ku Turo anatuma anyamata ace kwa Solomo, popeza anamva kuti adamdzoza mfumu m'malo mwa atate wace; pakuti Hiramu adakondana ndi Davide masiku onse.
2 Ndipo Solomo anatumiza mau kwa Hiramu, nati,
3 Mudziwa inu kuti atate wanga Davide sanathe kumangira dzina la Yehova Mulungu wace nyumba, cifukwa ca nkhondo zakumzinga konseko, mpaka atawaika Yehova pansi pa mapazi ace.
4 Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipumulitsa ku mbali zonse; palibe wotsutsana nane, kapena coipa condigwera.
5 Ndipo taonani, ndikuti ndimangire dzina la Yehova Mulungu wanga nyumba, monga Yehova anauza atate wanga Davide, ndi kuti, Mwana wako ndidzamuika pa mpando wako wacifumu m'malo mwako, iyeyo adzamangira dzina langa nyumbayo.
6 Ndipo tsono, lamulirani kuti anditemere mitengo yamkungudza ku Lebano, ndipo akapolo anga adzakhala ndi akapolo anu, ndipo ndidzakupatsani mphotho ya akapolo anu monga mudzanena; popeza mudziwa kuti pakati pa ife palibe mmisiri wakudziwa kutema mitengo ngati anthu a ku Sidoni.
7 Ndipo kunacitika, pamene Hiramu anamva mau ace a Solomo, anakondwera kwakukuru, nati, Alemekezeke Yehova lero amene wampatsa Davide mwana wanzeru akhale mfumu ya anthu aunyinji amenewa.
8 Ndipo Hiramu anatumiza kwa Solomo, nati, Ndazimva zija munatumiza kwa inezo, ndidzacita cifuniro canu conse, kunena za mitengo yamkungudza ndi mitengo yamlombwa.
9 Akapolo anga adzatsika nayo ku Lebano kufika nayo ku nyanja yamcere, ndipo ine ndidzaiyandamitsa paphaka kufikira komwe mudzandiuzako, ndi kumeneko ndidzaimasula, ndipo mudzaitenga; nimudzacita cifuniro canga, kumapatsa banja langa zakudya.
10 Tsono Hiramu anapatsa Solomo mitengo yamkungudza ndi mitengo yamlombwa monga momwe anafuniramo.
11 Ndipo Solomo anapatsa Hiramu miyeso ya tirigu zikwi makumi awiri ndiyo zakudya za banja lace, ndi miyeso makumi awiri ya mafuta oyera; motero Solomo anapatsa Hiramu caka ndi caka.
12 Ndipo Yehova anapatsa Solomo nzeru monga momwe adamlonjezera; ndipo panali mtendere pakati pa Hiramu ndi Solomo, iwo awiri napangana pamodzi.
13 Ndipo mfumu Solomo anasonkhetsa athangata mwa Aisrayeli onse, ndi athangatawo ndiwo anthu zikwi makumi atatu.
14 Ndipo anawatuma ku Lebano mwezi umodzi zikwi khumi kuwasintha, mwezi umodzi iwo anali ku Lebano, miyezi iwiri anali kwao; ndipo Adoniramu anali kapitao wa athangata.
15 Ndipo Solomo anawasenzetsa akatundu anthu zikwi makumi asanu ndi awiri, ndi anthu zikwi makumi asanu ndi atatu anatema m'mapiri;
16 osawerenga akapitao a Solomo akuyang'anira nchito, ndiwo zikwi zitatu mphambu mazana atatu, amenewo analamulira anthu aja akugwira nchito.
17 Ndipo mfumu inalamula iwo, natuta miyala yaikuru-ikuru ya mtengo wapatali, kuika maziko ace a nyumbayo ndi miyala yosemasema.
18 Ndipo omanga nyumba a Solomo ndi omanga nyumba a Hiramu ndi anthu a ku Gebala anaisema, naikonza mitengo ndi miyala yakumangira nyumbayo.
1 Ndipo kunacitika zitapita zaka mazana anai mphambu makumi asanu ndi atatu ataturuka ana a Israyeli m'dziko la Aigupto, caka cacinai cakukhala Solomo mfumu ya Israyeli, m'mwezi wa Zivi, ndiwo mwezi waciwiri, iye anayamba kumanga nyumba ya Yehova.
2 Ndipo nyumbayo mfumu Solomo anaimangira Yehova, m'litali mwace munali mikono makumi asanu ndi limodzi, ndi m'mimba mwace mikono makumi awiri, ndi msinkhu wace mikono makumi atatu.
3 Ndipo anamanga likole pakhomo pa nyumba ya kacisiyo, m'litali mwace munali mikono makumi awiri monga m'mimba mwace mwa nyumbayo, kupingasa kwace kunali mikono khumi ku khomo la nyumba.
4 Ndipo m'nvumbamo anamanga mazenera a made okhazikika.
5 Ndipo anamanga zipinda zosanjikizana zogundana ndi khoma, kuzungulira makoma a nyumba ya Kacisi, ndi monenera momwemo; namanga zipinda zozinga,
6 Cipinda capansico kupingasa kwace kunali mikono isanu, capakatico kupingasa kwace mikono isanu ndi umodzi, cacitatuco kupingasa kwace mikono isanu ndi iwiri; pakuti kubwalo anacepsa khoma pozungulirapo, mitanda isalongedwe m'makoma a nyumba.
7 Ndipo nyumbayo pomangidwa inamangidwa ndi miyala yokonzeratu asanaitute; ndipo m'nyumbamo simunamveka: kulira nyundo, kapena nkhwangwa, kapena cipangizo cacitsulo, pomangidwa iyo.
8 Khomo lolowera m'zipinda za pakati linali ku mbali ya ku dzanja lamanja ya nyumba; ndipo anthu amakwerera pa makwerero ozunguniza, kutikira ku zipinda za pakati, ndi kuturuka m'zapakatizo kulowa m'zacitatuzo,
9 Momwemo anamanga nyumbayo naitsiriza, naika mitanda, naifolera ndi matabwa amikungudza.
10 Ndipo anamanga zipindazo zogundana ndi nyumba yonseyo, cipinda ciri conse msinkhu wace mikono isanu; ndipo anazilumikizitsa kunyumba ndi mitengo yamkungudza.
11 Ndipo mau a Yehova anafika kwa Solomo, nati,
12 Kunena za nyumba yino ulikuimanga, ukamayenda iwe m'malemba anga, ndi kumacita maweruzo anga, ndi kumasunga malamulo anga onse kuyendamo, pamenepo Ine ndidzakhazikitsira iwe mau anga amene ndinauza Davide atate wako.
13 Ndipo ndidzakhala pakati pa ana a Israyeli osawasiya anthu anga a Israyeli.
14 Tsono Solomo anamanga nyumbayo naitsiriza.
15 Ndipo anacinga makoma a nyumba m'katimo ndi matabwa amkungudza, kuyambira pansi kufikira posanja, nacinga m'katimo ndi matabwa, nayala pansi m'nyumbamo matabwa amlombwa.
16 Ndipo anadulitsa ndi matabwa amkungudza mikono makumi awiri m'kati mwa nyumba m'tsogolo mwace, kuyambira pansi kulekeza kumitanda; ici anamanga m'katimo cikhale monenera, malo opatulikitsa.
17 Ndipo nyumbayo, ndiyo Kacisi wa cakuno ca monenera, inali ya mikono makumi anai.
18 Ndipo m'kati mwa nyumba munali mikungudza yosemasema, ngati zikho ndi maluwa oti gada; munali mikungudza yokha yokha simunaoneka mwala ai,
19 Ndipo anakonza monenera m'kati mwa nyumba m'tsogolo mwace, kuikamo likasa la cipangano la Yehova.
20 Ndipo m'kati mwa monenera m'menemo, m'litali mwace munali mikono makumi awiri, kupingasa kwace mikono makumi awiri, ndi msinkhu wace mikono makumi awiri; ndipo anamukuta ndi golidi woyengetsa, nakutanso guwa la nsembe ndi matabwa amkungudza,
21 Momwemo Solomo anakuta m'kati mwa nyumba ndi golidi woyengetsa, natambalika maunyolo agolidi cakuno ca monenera, namukuta ndi golidi.
22 Ndipo nyumba yonse anaikuta ndi golidi mpaka adatha nyumba yonse, ndi guwa lonse la nsembe linali cakuno ca monenera analikuta ndi golidi.
23 Ndipo m'moneneramo anasema mitengo yaazitona akerubi awiri, yense wa msinkhu wace mikono khumi.
24 Ndipo phiko limodzi la kerubi linali la mikono isanu, ndi phiko lina la kerubi linalinso la mikono isanu; kuyambira ku nsonga ya phiko limodzi kufikira ku nsonga ya phiko lina inali mikono khumi.
25 Ndi kerubi winayo msinkhu wace unali mikono khumi; akerubi onse awiri anafanana muyeso wao ndi msinkhu wao.
26 Msinkhu wa kerubi mmodzi unali mikono khumi, ndi wa kerubi wina momwemo.
27 Ndipo anaika akerubiwo m'cipinda ca m'katimo, ndi mapiko a akerubiwo anatambasuka kotero kuti phiko lace la kerubi mmodzi linajima ku khoma limodzi, ndipo phiko la kerubi wina linajima khoma lina, ndi mapiko ao anagundana pakati pa nyumba.
28 Ndipo anawakuta akerubi ndi golidi.
29 Nalemba m'makoma onse akuzinga cipinda mafano olemba ngati akerubi ndi migwalangwa ndi maluwa oti gada, m'katimo ndi kumbuyo kwace.
30 Ndipo anakuta ndi golidi pansi pace pa nyumba m'katimo ndi kunja.
31 Ndipo pa khomo la monenera anapanga zitseko za mtengo waazitona, citando ca khomolo cinali limodzi la magawo asanu a khoma lace.
32 Zitseko ziwiri zomwe zinali za mtengo waazitona, anasemapo ngati akerubi ndi migwalangwa ndi maluwa oti gada, nawakuta ndi golidi; inde anakutanso ndi golidi akerubi ndi migwalangwayo.
33 Momwemo anapanganso mphuthu zaazitona za pa khomo la Kacisi, citando cace cinali limodzi la magawo anai a khoma;
34 ndi zitseko ziwiri za mitengo yamlombwa pa khomo lina; panali citseko copatukana, ndi pa linzace panali citseko copatukana,
35 Ndipo analembapo ngati akerubi ndi migwalangwa ndi maluwa oti gada, nakuta zolembazo ndi golidi wopsyapsyala,
36 Ndipo bwalo la m'kati analimanga mizere itatu ya miyala yosemasema, ndi mzere umodzi wa mitanda yamkungudza.
37 Maziko ace a nyumba ya Mulungu anaikidwa m'caka cacinai m'mwezi wa Zivi.
38 Ndipo m'caka cakhumi ndi cimodzi m'mwezi wa Buli ndiwo mwezi wacisanu ndi citatu anatsiriza nyumba konse konse monga mwa mamangidwe ace onse. Momwemo anaimanga zaka zisanu ndi ziwiri.
1 Koma nyumba ya iye yekha Solomo anaimanga zaka khumi mphambu zitatu, natsiriza nyumba yace yonse.
2 Anamanganso nyumba yochedwa Nkhalango ya Lebano, m'litali mwace munali mikono zana limodzi, kupingasa kwace mikono makumi asanu, ndi msinkhu wace mikono makumi atatu; naisanja pa mizere inai ya mapanda amkungudza, ndi mitanda yamkungudza yotanthalika mapandawo.
3 Ndipo inayalidwa ndi mkungudza pamwamba pa zipinda makumi anai mphambu zisanu zolongosoledwa pa mapanda, mzere umodzi zipinda khumi mphambu asanu.
4 Ndipo panali mazenera m'mizere itatuyo, zenera limodzi lopenyana ndi linzace mizere itatu.
5 Ndipo makomo onse ndi mphuthu zonse zinali zamphwamphwa maonekedwe ace, ndipo zenera limodzi linapenyana ndi linzace mizere Itatu.
6 Ndipo anamanga khumbi la nsanamira, m'litali mwace munali mikono makumi asanu, kupingasa kwace mikono makumi atatu; ndipo panali khumbi lina patsogolo pace, ndi nsanamira ndi mitanda patsogolo pacepo.
7 Ndipo anamanga khumbi la mpando wacifumu loweruziramo iye, ndilo khumbi la mirandu, ndipo linayalidwa ndi mkungudza pansi ndi posanja.
8 Ndipo nyumba yace yakukhalamo iye, m'bwalo lina la m'tsogolo mwa khumbilo, linamangidwa cimodzimodzi. Anammangiranso nyumba mwana wamkazi wa Farao, amene adamkwatira Solomo, yofanafana ndi khumbi limeneli.
9 Izi zonse zinali za miyala ya mtengo wapatali yosemasema, ya muyeso muyeso, yoceka ndi mipeni ya mano mana m'katimo ndi kunjako, kuyambira kumazikokufikira kumutu, momwemonso kunjako ku bwalo lalikuru,
10 Ndipo maziko ace anali a miyala ya mtengo wapatali, ndiyo miyala yaikulu, miyala ya mikono khumi, ndi miyala ya mikono isanu ndi itatu.
11 Ndi pamwamba pace panali miyala ya mtengo wapatali, ndiyo miyala yosemasema monga muyeso wace, ndi mitengo yamkungudza.
12 Ndipo bwalo lalikuru lozingapo linali ndi mizere itatu ya miyala yosemasema, ndi mzere umodzi wa mitanda yamkungundza, monga bwalo la pakati pa nyumba ya Yehova, ndi likole la nyumbayo.
13 Ndipo mfumu Solomo anatuma anthu kukatenga Hiramu ku Turo.
14 Iyeyo anali mwana wace wa mkazi wamasiye wa pfuko la Nafitali, atate wace anali munthu wa ku Turo, mfundi wa mkuwa; ndipo iye anadzala ndi nzeru ndi luntha ndi luso kugwira nchito zonse za mkuwa. Ndipo anadza kwa mfumu Solomo namgwirira nchito zace zonse.
15 Popeza iyeyu anaunda nsanamira ziwiri zamkuwa, msinkhu wace wa imodzi unali mikono khumi mphambu isanu ndi itatu; ndipo cingwe ca mikono khumi mphambu iwiri cinayesa thupi la nsanamira imodzi.
16 Ndipo anapanga mitu iwiri ya mkuwa wosungunula, kulika pamwamba pa nsanamirazo, msinkhu wace wa mutu wina unali mikono isanu, ndi msinkhu wa mutu unzace mikono isanu.
17 Ndipo panali maukonde olukaluka ndi zoyangayanga, zokolana za pa mitu imene inali pamwamba pa nsanamira; zisanu ndi ziwiri za pa mutu wina, ndi zisanu ndi ziwiri za pa mutu unzace.
18 M'mwemo anapanga nsanamira, ndipo panali mizere iwiri yozungulira ukonde umodzi, kukuta ndi makangaza mituyi inali pamwambapo, nacita momwemo ndi mutu winawo.
19 Ndipo mituyi inali pamwamba pa nsanamira za pa likole inali ngati akakombo malembedwe ace, a mikono inai.
20 Ndipo panalinso mitu pamwamba pa nsanamira ziwirizo, pafupi pa mimbayo, inali m'mbali mwace mwa ukondewo; ndipo makangazawo anali mazana awiri, akukhala mizere yozinga nda nda mutu winawo.
21 Ndipo anaimiritsa nsanamirazi pa likole la Kacisi; naimiritsa nsanamira ya ku dzanja lamanja, nacha dzina lace Yakini; naimiritsa nsanamira yakumanzere, nacha dzina lace Boazi.
22 Ndipo pamwamba pa nsanamirazo panali ngati akakombo malembedwe ace; motero anaitsiriza nchito ya nsanamirazo.
23 Ndipo anayenganso thawale lamkuwa, kukamwa kwace kunali kwa mikono khumi, linali lozunguniza, ndi msinkhu wace unali mikono isanu; ndi cingwe ca mikono makumi atatu cinalizungulira.
24 Ndipo m'khosi mwace munali ngati zikho zozinganiza m'mkono umodzi zikho khumi zakuzinganiza thawalelo; zikhozo zinayengedwa m'mizere iwiri poyengedwa thawalelo.
25 Linasanjikika pa ng'ombe khumi mphambu ziwiri, zitatu zinapenya kumpoto, zitatu kumadzulo, zitatu kumwera, zitatu kum'mawa; ndipo thawalelo linakhazikika pamwamba pa izo; ndipo nkholo zao zinayang'anana.
26 Ndipo kucindikira kwace kunali ngati m'manja mwa munthu, ndipo mlomo wace unasadamuka ngati mlomo wa comwera, ngati maluwa akakombo, analowamo madzi a mitsuko yaikuru zikwi ziwiri.
27 Ndipo anapanga maphaka khumi amkuwa, m'litali mwace mwa phaka limodzi mikono inai, ndi kupingasa kwace mikono inai, ndi msinkhu wace mikono itatu.
28 Ndipo mapangidwe a maphakawo anali otere: anali nao matsekerezo ao, ndipo matsekerezo anali pakati pa mbano.
29 Ndipo pa matsekerezo a pakati pa mbano panali ngati mikango ndi ng'ombe ndi akerubi, ndi pamwamba pa mbano panali cosanjikirapo; ndipo pansi pa mikango ndi ng'ombe panaphatikizika zotsetseremba zoyangayanga zokoloweka.
30 Ndipo phaka lid lonse linali ndi njinga zamkuwa zinai ndi mitanda yamkuwa, ndipo ngondya zace zinai zinali ndi mapewa; pansi pa thawale panali mapewa oyengeka pa mbali pa zophatikizika zonse.
31 Ndipo pakamwa pace m'katimo pamwamba pa cosanjikira, panayesa mkono umodzi; koma pakamwa pace panali posadamuka, monga mapangidwe ace a cosanjikira, mkono umodzi ndi nusu; ndiponso pakamwa pace panali zolemba ndi matsekerezo ace anali amphwamphwa, si ozunguniza.
32 Ndipo njinga zinai zinali pansi pa matsekerezo, ndi mitanda ya njinga inali m'mphakamo, ndi msinkhu wa njinga imodzi unali mkono umodzi ndi nusu.
33 Ndipo mapangidwe a njinga analingana ndi mapangidwe a njinga za gareta, mitanda yace ndi mkombero wace ndi nthiti zace ndi mtima wace zonsezo zinayengedwa.
34 Ndipo panali ngati mapewa anai pansi pa ngondya zinai za phaka limodzi, mapewawo anali a phaka lomwelo.
35 Ndipo pamwamba pa phaka panali khoma lozunguniza, msinkhu wace nusu ya mkono; ndi pamwamba pa phaka panali mbano zace ndi matsekerezo a phaka lomwelo.
36 Ndipo m'mapanthi mwa mbano zace ndi pa matsekerezo ace analemba ngati akerubi ndi mikango ndi migwalangwa, monga mwa malo ace a zonsezo, ndi zoyangayanga zozungulira.
37 Motero anapanga maphaka khumiwo, anafanana mayengedwe ao muyeso wao ndi maonekedwe ao.
38 Ndipo anapanga mbiya zamphwamphwa khumi zamkuwa; m'mbiya imodziyo munalowamo madzi a mitsuko yaikuru makumi anai, ndipo mbiya iri yonse inali ya mikono inai: pa phaka liri lonse la maphaka aja khumi panakhala mbiya imodzi.
39 Ndipo anaika maphaka asanu ku dzanja lamanja la nyumba, ndi maphaka asanu ku dzanja lamanzere la nyumba; naika thawalelo ku dzanja lamanja la nyumba kum'mawa kupenya kumwera.
40 Ndipo Hiramu anayenga mbiyazo ndi zoolera ndi mbale zowazira. Motero Hiramu anatsiriza kupanga nchito yonse anaicitira mfumu Solomo ya m'nyumba ya Yehova.
41 Nsanamira ziwirizo, ndi mbale za mitu inali pamwamba pa nsanamira ziwirizo, ndi maukonde awiri ophimbira mbale ziwiri za mitu inali pamwamba pa nsanamirazo,
42 ndi makangaza mazana anai a maukonde awiriwo, mizere iwiri ya makangaza a ukonde umodzi kuphimbira mbale ziwiri za mitu inali pa nsanamirazo,
43 ndi maphaka khumiwo ndi mbiya khumi ziri pa maphakawo,
44 ndi thawale limodzilo, ndi ng'ombe khumi mphambu ziwirizo pansi pa thawale;
45 ndi miphikayo, ndi zoolerazo, ndi mbalezo; inde zotengera zonse zimene Hiramu anampangira mfumu Solomo za m'nyumba ya Yehova, zinali za mkuwa wonyezimira.
46 Mfumu inaziyenga pa cidikha ca ku Yordano, m'dothe ladongo, pauti pa Sukoti ndi Zaritani.
47 Ndipo Solomo anazileka zipangizo zonse osaziyesa, popeza zinacuruka ndithu; kulemera kwace kwa mkuwa wonsewo sikunayeseka.
48 Ndipo Solomo anapanga zipangizo zonse za m'nyumba ya Mulungu: guwa la nsembe lagolidi, ndi gome lagolidi loikapo mikate yoonekera;
49 ndi zoikapo nyali za golidi woyengetsa, zisanu ku dzanja lamanja, zisanu kulamanzere, cakuno ca monenera, ndi maluwa ndi nyali ndi mbano zagolidi;
50 ndi zikho, ndi zozimira nyali, ndi mbale, ndi zipande, ndi zopalira mota za golidi woyengetsa, ndi zomangira zitseko zagolidi, za zitseko za cipinda ca m'katimo, malo opatulikitsa, ndiponso za zitseko za nyumba ya Kacisi.
51 Motero nchito zonse zinatsirizika, zimene mfumu Solomo anacitira nyumba ya Yehova. Ndipo Solomo analonga zinthu adazipatula Davide atate wace, ndizo siliva ndi golidi ndi zipangizo zomwe naziika mosungira cuma ca nyumba ya Yehova.
1 Pamenepo Solomo anasonkhanitsa akulu a Israyeli, ndi akulu onse a mafuko, akalonga a nyumba za atate a ana a Israyeli, kwa mfumu Solomo m'Yerusalemu, kukatenga likasa la cipangano ca Yehova m'mudzi wa Davide, ndiwo Ziyoni.
2 Ndipo anthu onse a Israyeli anasonkhana kwa mfumu Solomo kukadyereram'mwezi wa Etanimu, ndiwo mwezi wacisanu ndi ciwiri.
3 Ndipo akulu onse a Israyeli anadza, ansembe nanyamula likasa.
4 Ndipo anatenga likasa la Yehova, ndi cihema cokomanako, ndi zipangizo zonse zopatulika, zinali m'cihemamo, inde zimenezi anazitenga ansembe ndi Alevi.
5 Ndipo mfumu Solomo ndi msonkhano wonse wa Israyeli wosonkhana kwa iye anali naye kulikasa, naphera nkhosa ndi ng'ombe za nsembe zosawerengeka ndi zosadziwika, cifukwa ca unyinji wao.
6 Ndipo ansembe analonga likasa la cipangano ca Yehova kumalo kwace, ku monenera mwa nyumba, ku malo opatulikitsa, munsi mwa mapiko a akerubi,
7 Popeza akerubiwo anatambasula mapiko ao awiri pamwamba pa likasa, ndipo akerubiwo anaphimba pamwamba pa likasa ndi mphiko zace.
8 Ndipo mphikozo zinatalika kuti nsonga za mphiko zidaoneka ku malo opatulika cakuno ca monenera; koma sizinaoneka kubwalo; ndipo zikhala pomwepo mpaka lero lino.
9 Munalibe kanthu m'likasamo koma magome awiri aja amwala Mose anawalongamo pa Horebu, pamene Yehova anapangana ndi ana a Israyeli, poturuka iwo m'dziko la Aigupto.
10 Ndipo kunacitika ataturuka ansembe m'malo opatulika, mtambo unadzaza nyumba ya Yehova,
11 ndipo ansembe sanakhoza kuimirira kurumikira cifukwa ca mtambowo, popeza ulemerero wa Yehova unadzazanyumba ya Yehova.
12 Pamenepo Solomo anati, Yehova ananena kuti adzakhala m'mdima waukuru.
13 Ine ndakumangirani ndithu nyumba yokhalamo Inu, ndiyo malo okhalamo inu nthawi zosatha.
14 Ndipo mfumu inapotoloka nkhope yace, nidalitsa msonkhano wonse wa Israyeli, Ndi msonkhano wonse wa Israyeli unaimirira.
15 Nati iye, Wolemekezeka ndi Yehova Mulungu wa Israyeli amene analankhula m'kamwa mwace ndi Davide atate wanga, nakwaniritsa ndi dzanja lace, nati,
16 Kuyambira tsiku lakuturutsa Ine anthu anga Aisrayeli m'dziko la Aigupto, sindinasankha mudzi uli wonse mwa mafuko onse a Israyeli kumangamo nyumba yokhalamo dzina langa, koma ndinasankha Davide kukhala mfumu ya anthu anga Aisrayeli.
17 Ndipo Davide atate wanga anafuna m'mtima mwace kumangira dzina la Yehova Mulungu wa Israyeli nyumba.
18 Koma Yehova ananena ndi Davide atate wanga, Popeza unafuna m'mtima mwako kumangira dzina langa nyumba, unacita bwino kuti m'mtima mwako unatero.
19 Koma usamange ndiwe nyumbayo, koma mwana wako adzaturuka m'cuuno mwako, iyeyo adzamangira dzina langa nyumba.
20 Ndipo Yehova wakhazikitsa mau ace analankhulawo, ndipo ndauka ndine m'malo mwa Davide atate wanga, ndipo ndikhala pa mpando wacifumu wa Israyeli monga adalonjeza Yehova, ndipo ndamangira dzina la Yehova Mulungu wa Israyeli nyumba.
21 Ndipo ndakonzera malo likasalo, m'mene muli cipangano ca Yehova, cimene anapangana ndi makolo athu pamene anawaturutsa m'dziko la Aigupto.
22 Ndipo Solomo anaimirira ku guwa la nsembe la Yehova pamaso pa msonkhano wonse wa Israyeli, natambasulira manja ace kumwamba, nati,
23 Yehova Mulungu wa Israyeli, palibe Mulungu wolingana ndi inu m'thambo la kumwamba, kapena pa dziko lapansi, wakusungira cipangano ndi cifundo akapolo anu akuyenda ndi mtima wonse pamaso panu,
24 wakusungira mtumild wanu Davide atate wanga cimene mudamlonjezaco; munalankhulanso m'kamwa mwanu ndi kukwaniritsa ndi dzanja lanu monga lero lino.
25 Ndipo tsopano, Yehova Mulungu wa Israyeli, msungireni mtumiki wanu Davide atate wanga cimene cija mudamlonjezaco, ndi kuti, Sadzakusowa munthu pamaso panga wokhala pa mpando wacifumu wa Israyeli; komatu ana ako acenjere njira yao, kuti akayende pamaso panga monga umo unayendera iwe pamaso panga.
26 Ndipo tsopano, Mulungu wa Israyeli, atsimikizike mau anu amene munalankhula ndi mtumiki wanu Davide atate wanga.
27 Kodi Mulungu adzakhala ndithu pa dziko lapansi? Taonani, thambo ndi m'Mwambamwamba zicepa kukulandirani, koposa kotani nanga nyumba iyi ndaimangayi.
28 Koma muceukire pemphero la kapolo wanu, ndi pembedzero lace, Yehova Mulungu wanga, kumvera kulira ndi kupempha kwace kumene kapolo wanu apempha pamaso panu lero;
29 kuti maso anu atsegukire nyumba yino usiku ndi usana, kumalo kumene munanenako, Dzina langa lidzakhala komweko; kuti mumvere pemphero limene adzapemphera kapolo wanu lolunjika kumalo kuno.
30 Ndipo mverani pembedzero la kapolo wanu ndi la anthu anu Aisrayeli, pamene adzapemphera molunjika kumalo kuno; ndipo mverani Inu m'Mwamba mokhala Inumo; ndipo pamene mukumva, khululukirani.
31 Ngati munthu akacimwira mnzace, ndi lumbiro likaikidwa pa iye kumlumbiritsa, ndipo akadzalumbira patsogolo pa guwa la nsembe lanu m'nyumba yino;
32 mverani Inu pamenepo m'mwambamo, ndipo citani, weruzani akapolo anu, kumtsutsa woipayo, ndi kumbwezera cimo lace, ndi kulungamitsa wolungamayo kumbwezera monga cilungamo cace.
33 Ndipo anthu anu Aisrayeli akawakantha adani ao cifukwa ca kucimwira Inu, ndipo akabweranso kwa Inu, lodi kubvomereza dzina lanu, ndi kupemphera, ndi kupembedza Inu m'nyumba muno;
34 pamenepo mverani Inu m'Mwambamo, ndi kukhululukira cimo la anthu anu Aisrayeli, ndi kuwabwezera ku dziko limene munapatsa makolo ao.
35 Pamene kumwamba kwatsekeka, ndipo kulibe mvula cifukwa ca kucimwira Inu, nakapemphera iwo molunjika kumalo kuno, ndi kubvomereza dzina lanu, ndi kutembenuka kusiya zoipa zao, pakuwasautsa Inu;
36 pamenepo mverani Inu m'Mwamba, ndi kukhululukira cimo la akapolo anu, ndi la, anthu anu Aisrayeli; pakuti muwaphunzitsa njira yokoma ayenera kuyendamo, ndi kupatsa mvula pa: dziko lanu, limene munawapatsa anthu anu likhale colowa cao.
37 M'dziko mukakhala odala, mukakhala mliri, mlaza, cinoni, dzombe, kapena kapuci, adani ao akawamangira misasa m'dziko la midzi yao, mukakhala mliri uti wonse, kapena nthenda;
38 tsono pempho ndi pembedzero liri lonse akalipempha munthu ali yense, kapena anthu anu onse Aisrayeli, pakuzindikira munthu yense cinthenda ca mtima wa iye yekha, ndi kutambasulira manja ace ku nyumba yino;
39 pamenepo mverani Inu m'Mwamba mokhala Inu, ndi kukhululukira, ndi kucita, ndi kubwezera munthu yense monga njira zace zonse, amene Inu mumdziwa mtima wace, popeza Inu, Inu nokha, mudziwa mitima ya ana onse a anthu;
40 kuti aope Inu masiku onse akukhala iwowo m'dziko limene Inu munapatsa makolo ao.
41 Ndiponso kunena za mlendo, wosati wa anthu anu Aisrayeli, koma wakufumira m'dziko lakutali cifukwa ca dzina lanu,
42 popeza adzamva za dzina lanu lalikuru ndi dzanja lanu lamphamvu ndi mkono wanu wotambasuka; akabwera iyeyo nadzapemphera molunjika ku nyumba yino;
43 mverani Inu m'Mwamba mokhala Inu, ndipo citani monga mwa zonse mlendoyo azipempha kwa Inu; kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu, kuopa Inu, monga amatero anthu anu Aisrayeli, ndi kuti adziwe kuti nyumba yino ndaimangayi yachedwa dzina lanu.
44 Akaturuka anthu anu kukayambana nkhondo ndi adani ao, kumene konse inu mudzawatuma, ndipo akapemphera kwa Yehova molunjika ku mudzi uno munausankha Inu, ndi ku nyumba ndamangira dzina lanu;
45 pamenepo mverani Inu m'Mwamba pempho ndi pembedzero lao, ndi kulimbitsa mlandu wao.
46 Akacimwira Inu, popeza palibe munthu wosacimwa, ndipo mukakwiya nao ndi kuwapereka kwa adani, kuti iwo awatenge ndende kumka nao ku dziko la adani, ngati kutali kapena kufupi,
47 ndipo akakumbukila mitima yao, ali kudziko kumene anatengedwa ukapolo, nakalapa, nakapembedza inu m'dziko la iwo anawatenga ndende, ndi kuti, Tacimwa, ndipo tacita mphulupulu, tacita moipa;
48 ndipo akabwerera kwa Inu ndi mtima wao wonse ndi moyo wao wonse, m'dziko la adani ao adawatenga ndendewo, ndipo akapemphera kwa Inu molunjika ku dziko lao munapatsa makolo aolo, ku mudzi munausankha Inu, ndi kunyumba ndamangira dzina lanu;
49 pamenepo mverani Inu pemphero ndi pembedzero lao m'Mwamba mokhala Inumo, ndi kulimbitsa mlandu wao,
50 ndi kukhululukira anthu anu adacimwira Inu ndi mphulupulu zao zonse adaparamula nazo kwa Inu; ndipo muwacititsire cifundo iwo amene anawagwira ndende, kuti awacitire cifundo;
51 pakuti awa ndi anthu anu ndithu, ndi colowa canu cimene munaturutsa m'Aigupto, m'kati mwa ng'anjo ya citsulo;
52 kuti maso anu akatsegukire pembedzero la kapolo wanu ndi pembedzero la anthu anu Aisrayeli, kuwamveram'menemonseakapfuula kwa Inu.
53 Popeza Inu munawapatula pa anthu onse a pa dziko lapansi akhale colowa canu, monga munanena ndi dzanja la Mose mtumiki wanu, pamene munaturutsa makolo athu m'Aigupto, Yehova Mulungu Inu.
54 Ndipo kunali kuti atatsiriza Solomo kupemphera kwa Yehova pemphero ndi pembedzero lino lonse, ananyamuka ku guwa la nsembe la Yehova pomwe analikugwada pa mabondo ace, ndi manja ace otambasulira kumwamba.
55 Naimirira, nadalitsa msonkhano wonse wa Israyeli ndi mau okweza, nati,
56 Wolemekezeka ndi Yehova amene anapumulitsa anthu ace Aisrayeli, monga mwa zonse analonjezazo; sanatayika mau amodzi a mau ace onse abwino, amene analankhula ndi dzanja la Mose mtumiki wace.
57 Yehova Mulungu wathu akhale nafe monga umo anakhalira nao makolo athu, asatisiye kapena kutitaya;
58 kuti atitembenuzire kwa iye yekha mitima yathu iyende m'njira zace zonse, ndi kusunga malamulo ace onse ndi malemba ace ndi maweruzo ace, amene anawalamulira makolo athu.
59 Ndipo mau anga amenewa ndapembedzera nao pamaso pa Yehova akhale pafupi ndi Yehova Mulungu wathu usana ndi usiku, kuti alimbitse mlandu wa kapolo wace, ndi mlandu wa anthu ace Aisrayeli, mlandu wa tsiku pa tsiku lace;
60 kuti anthu onse a pa dziko lapansi akadziwe kuti Yehova ndiye Mulungu, palibe wina.
61 Mitima yanu ikhale yangwiro ndi Yehova Mulungu wathu, kuyenda m'malemba ace ndi kusunga malamulo ace, monga lero lino.
62 Ndipo mfumu ndi anthu onse a Israyeli pamodzi naye anaphera nsembe pamaso pa Yehova.
63 Ndipo Solomo anaphera nsembe yamtendere, yophera kwa Yehova ng'ombe zikwi makumi awiri mphambu ziwiri, ndi nkhosa zikwi zana limodzi mphambu makumi awiri. Momwemo mfumu ndi ana a Israyeli onse anapereka nyumbayo ya Yehova.
64 Tsiku lomwelo mfumu inapatulira Mulungu pakati pace pa bwalo la ku khomo la nyumba ya Yehova; pakuti pomwepo anapereka nsembe yopsereza ndi nsembe yaufa, ndi mafuta a nsembe zamtendere; popeza guwa la nsembe lamkuwa linali pamaso pa Yehova lidacepa kulandira nsembe zopsereza, ndi nsembe zaufa, ndi mafuta a nsembe zamtendere.
65 Ndipo nthawi yomweyo Solomo anacita madyerero pamaso pa Yehova Mulungu wathu, ndi Israyeli yense pamodzi naye, msonkhano waukuru wakuyambira polowera ku Hamati kufikira ku nyanja ya ku Aigupto, masiku asanu ndi awiri, ndi masiku asanu ndi awiri ena, ndiwo masiku khumi mphambu anai.
66 Tsiku lacisanu ndi citatu anawauza anthu apite; ndipo iwo anadalitsa mfumu, napita ku mahema ao osekera ndi okondwera mtima cifukwa ca zokoma zonse Yehova anacitira Davide mtumiki wace, ndi Israyeli anthu ace.
1 Ndipo kunali, atatsiriza Solomo kumanga nyumba ya Yehova, ndi nyumba ya mfumu, ndi cifuniro conse ca Solomo anacikhumbaco,
2 Yehova anaonekera kwa Solomo nthawi yaciwiri, monga momwe adamuonekera ku Gibeoni.
3 Ndipo Yehova anati kwa iye, Ndamva pemphero lako ndi pembedzero lako wandipembedza nalo; ndapatula nyumba imene waimangayi kuikamo dzina langa nthawi zosatha, ndipo maso anga ndi mtima wanga zidzakhala kumeneko masiku onse.
4 Ndipo iwe ukadzayenda pamaso panga, monga momwe Davide atate wako anayendera ndi mtima woona ndi wolungama, kuzicita zonse ndakulamulirazo, ndi kusunga malemba anga ndi maweruzo anga,
5 pamenepo Ine ndidzakhazikitsa cimpando ca ufumu wako pa Israyeli nthawi yosatha, monga ndinalonjezana ndi Davide atate wako, ndi kuti, Sadzakusowa munthu wamwamuna pa mpando wacifumu wa Israyeli.
6 Koma mukadzabwerera pang'ono pokha osanditsata, kapena inu, kapena ana anu, osasunga malamulo anga ndi malemba anga amene ndawaika pamaso panu; mukadzatumikira milungu yina ndi kuilambira;
7 pamenepo Ine ndidzalikha Aisrayeli kuwacotsera m'dziko ndidawapatsali; ndipo nyumba yino ndapatulira dzina langayi ndidzaitaya kosapenyeka; ndipo Israyeli adzakhala ngati mwambi ndi nkhani pakati pa anthu onse.
8 Ndipo munthu yense wopitirira pa nyumba yaitali yino adzadabwa nayo, nadzainyoza, nadzati, Yehova watero cifukwa ninji ndi dziko lino ndi nyumba yino?
9 Ndipo anthu adzayankha, Popeza anasiya Yehova Mulungu wao amene adaturutsa makolo ao m'dziko la Aigupto, natsata milungu yina, nailambira, naitumikira; cifukwa cace Yehova anawagwetsera coipa conseci.
10 Ndipo kunali, zitatha zaka makumi awiri m'mene Solomo adatsiriza nyumba ziwirizo, ndizo nyumba ya Yehova ndi nyumba ya mfumu;
11 popeza Hiramu mfumu ya Turo adamthandiza Solomo ndi mitengo yamkungudza ndi yamlombwa ndi golidi yemwe, monga momwe iye anafuniramo, cifukwa cace mfumu Solomo anampatsa Hiramu midzi makumi awiri m'dziko la Galileya.
12 Ndipo Hiramu anaturuka ku Turo kukaona midzi adampatsa Solomoyo, koma siinamkomera.
13 Nati, Midzi yino mwandipatsayi njotani, mbale wanga? Naicha dzina lao, Dziko lacikole, kufikira lero lino.
14 Ndipo Hiramu adatumiza kwa mfumu matalenti a golidi zana limodzi mphambu makumi awiri.
15 Ndipo cifukwa cace ca msonkho uja anausonkhetsa mfumu Solomo ndi cimeneci; kuti amange nyumba ya Yehova, ndi nyumba ya iye yekha, ndi Milo, ndi linga la Yerusalemu, ndi Hazori, ndi Megido; ndi Gezeri.
16 Pakuti Farao mfumu ya Aigupto adakwera nalanda Gezeri, nautentha ndi moto, nawapha Akanani akukhala m'mudzimo, naupereka kwaulere kwa mwana wace mkazi wa Solomo.
17 Ndipo Solomo anamanganso Gezeri, ndi Betihoroni wakunsi,
18 ndi Balati, ndi Tadimori wa m'cipululu m'dziko muja,
19 ndi midzi yonse yosungamo zinthu zace za Solomo, ndi midzi yosungamo magareta ace, ndi midzi yokhalamo apakavalo ace, ndi zina ziti zonse zidakomera Solomo kuzimanga m'Yerusalemu, ndi ku Lebano, ndi m'dziko lonse la ufumu wace.
20 Ndipo Aamori, ndi Ahiti, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi otsala, amene sanali a ana a Israyeli,
21 ana ao amene adatsala m'dziko, amene ana a lsrayeli sanakhoza kuononga konse, Solomo anawasenzetsa msonkho wa nchito kufikira lero.
22 Koma Solomo sanawayesa ana a Israyeli akapolo, koma iwowo anali anthu a nkhondo, ndi anyamata ace, ndi akalonga ace, ndi akazembe ace, ndi oyang'anira magareta ace ndi apakavalo ace.
23 Ameneyo anali akulu a akapitao oyang'anira nchito ya Solomo, mazana asanu mphambu makumi asanu akulamulira anthu ogwira nchito aja.
24 Koma mwana wamkazi wa Farao anaturuka m'mudzi wa Davide kukwera ku nyumba yace adammangira Solomo, pamenepo iye anamanganso Milo.
25 Ndipo caka cimodzi Solomo anapereka katatu nsembe zopsereza ndi zamtendere, pa guwa la nsembe limene anammangira Yehova, nafukiza zonunkhira pa guwa la nsembe pamaso pa Yehova, atatsiriza nyumbayo.
26 Ndipo mfumu Solomo anamanga zombo zambiri ku Ezioni Geberi uli pafupi ndi Eloti, pambali pa Nyanja Yofiira, ku dziko la Edomu.
27 Ndipo, Hiramu anatuma anyamata ace m'zombozo amarinyero ozerewera m'nyanja, pamodzi ndi anyamata a Solomo.
28 Ndipo iwo anafika ku Ofiri, natengako golidi matalenti mazana anai mphambu makumi awiri, nafika naye kwa mfumu Solomo.
1 Ndipo atamva mfumu yaikazi ya ku Seba mbiri ya Solomo yakubukitsa dzina la Yehova, anadza kumuyesera iye ndi miyambi yododometsa.
2 Nafika ku Yerusalemu ndi ulendo wace waukulu, ndi ngamila zakunyamula zonunkhira, ndi golidi wambiri, ndi timiyala ta mtengo wapatali; ndipo atafika kwa Solomo anakamba naye zonse za m'mtima mwace.
3 Ndipo Solomo anamyankha miyambi yace yonse, panalibe kanthu kobisika ndi mfumu kamene sanamfotozera iye.
4 Ndipo pamene mfumu yaikazi ya ku Seba adaona nzeru zonse za Solomo, ndi nyumba adaimangayo,
5 ndi zakudya za pa gome lace, ndi makhalidwe a anyamata ace, ndi maimiriridwe a atumiki ace, ndi zobvala zao, ndi otenga zikho ace, ndi nsembe yace yopsereza imene amapereka m'nyumba ya Yehova, anakhululuka malungo.
6 Ndipo anati kwa mfumu, idali yoonadi mbiri ija ndinaimva ine ku dziko langa ya macitidwe anu ndi nzeru zanu.
7 Koma sindinakhulupira mau amenewo mpaka ndafika ine kuno, ndaona ndi maso anga; ndipo taonani, anangondiuza dera lina lokha; nzeru zanu ndi zokoma zanu zakula pa mbiri ndinaimvayo.
8 Odala anthu anu, odala anyamata anu akukhala nthawi zonse pamaso panu, akumvaimva nzeru yanu.
9 Wolemekezeka Yehova Mulungu wanu amene anakondwera nanu, kukuikani pa mpando wacifumu wa Israyeli; popeza Yehova anakonda Israyeli nthawi yosatha, cifukwa cace anakulongani inu ufumu, kuti mucite ciweruzo ndi cilungamo.
10 Ndipo mkaziyo ananinkha mfumu matalenti a golidi zana limodzi mphambu makumi awiri, ndi zonunkhira zaunyinji, ndi timiyala ta mtengo wapatali; sunafikanso unyinji wotero wa zonunkhira wolingana ndi uja mfumu yaikazi inapereka kwa mfumu Solomo.
11 Ndipo zombe za Hiramu zotengera golidi ku Ofiri zinatenganso ku Ofiri mitengo yambiri yambawa, ndi timiyala ta mtengo wapatali.
12 Ndipo mfumu inasema mitengo yambawayo, ikhale mizati ya nyumba ya Yehova, ndi ya nyumba ya mfumu; ndiponso azeze ndi zisakasa za oyimbawo; siinafika kapena kuonekanso mpaka lero mitengo yotero yambawa.
13 Ndipo mfumu Solomo ananinkha mfumu yaikazi ya ku Seba cifuniro cace conse anacipempha iye, osawerenga cimene Solomo anamninkha mwa ufulu waceo Momwemo iye anabwerera namukanso ku dziko lace, iyeyo ndi anyamata ace.
14 Tsono kulemera kwace kwa golidi anafika kwa Solomo caka cimodzi kunali matalenti mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi liimodzi a golidi,
15 osawerenganso winayo wa anthu a malonda oyendayenda, ndi wa amalonda ena, ndi wa mafumu onse a Arabu, ndi wa akazembe onse a madera.
16 Ndipo mfumu Solomo anapanga zikopa mazana awiri zagolidi wonsansantha, cikopa cimodzi cinapangidwa ndi masekeli mazana asanu ndi limodzi.
17 Ndi malihawo mazana atatu a golidi wonsansantha, libawo limodzi linapangidwa ndi miyeso itatu ya golidi; ndipo mfumu inazisungira zonse m'nyumba yochedwa Nkhalango ya Lebano.
18 Ndipo mfumu inapanga mpando waukulu wacifumu waminyanga, naukuta ndi golidi woyengetsa.
19 Mpandowo wacifumu unali ndi makwerero asanu ndi limodzi, ndi pamwamba pa mpando wacifumu panali pozungulira kumbuyoko, ndipo munali ngati manja m'mbali zonse ziwiri za pokhalirapo, naimika mikango iwiri m'mbali mwa manjawo.
20 Ndipo anaimikamikango khumi ndi iwiri mbali yina ndi yina, pa makwerero asanu ndi limodzi aja; m'dziko liri lonse tina simunapangidwa wotere.
21 Ndipo zikho zomwera zonse za mfumu Solomo zinali zagolidi, ndi zotengera zonse za nyumba yochedwa Nkhalango ya Lebano zinali zagolidi yekha yekha, panalibe zasiliva, pakuti siliva ana ngoyesedwa opanda pace masiku onse a Solomo.
22 Popeza mfumu inali nazo panyanja zombo za ku Tarisi, pamodzi ndi zombo za Hiramu; zombo za ku Tarisi zinafika, kamodzi zitapita zaka zitatu, ziri nazo golidi, ndi siliva, ndi minyanga, ndi apusi, ndi mbalame za zitsukwa zazitali za maanga maanga.
23 Ndipo mfumu Solomo anawaposa mafumu onse a dziko lapansi pa cuma ndi nzeru.
24 Ndipo anthu onse a pa dziko anafuna nkhope ya Solomo, kudzamva nzeru zace zimene Mulungu analonga m'mtima mwace.
25 Ndipo akafika munthu yense ndi mtulo wace, zotengera zasiliva, ndi zotengera zagolidi, ndi zobvala, ndi zida, ndi zonunkhira, ndi akavalo, ndi nyuru; momwemo caka ndi caka.
26 Ndipo Solomo anasonkhanitsa, magareta ndi apakavalo; anali nao magareta cikwi cimodzi mphambu, mazana anai, ndi apakavalo zikwi khumi mphambu ziwiri, nawasungira m'midzi yosungamo magareta, ndi kwamfumu m'Yerusalemu.
27 Ndipo mfumu inacurukitsa siliva ngati miyala m'Yerusalemu, ndi mitengo yamikungudza anailinganiza ndi mikuyu ya m'madambo.
28 Ndipo akavalo a Solomo anacokera ku Aigupto; anthu a malonda a mfumu anawagula magulu magulu, gulu liri lonse mtengo wace.
29 Ndipo gareta limodzi linacokera kuturuka m'Aigupto mtengo wace masekeli a siliva mazana asanu ndi limodzi, ndi kavalo mtengo wace masekeli zana limodzi mphambu makumi asanu; momwemonso iwo anawagulira mafumu onse a Ahiti ndi mafumu a Aramu.
1 Ndipo mfumu Solomo anakonda akazi ambiri acilendo, pamodzi ndi mwana wamkazi wa Farao, akazi a ku Moabu, ndi a ku Amoni, ndi a ku Edomu, ndi a ku Zidoni, ndi Ahiti;
2 a mitundu ija Yehova adanena ndi ana a Israyeli za iwo, kuti, Inu musakalowa kwa iwo, ndipo iwo asadzalowe kwa inu; zedi adzatembenuza mitima yanu kutsata milungu yao; amenewo Solomo anawaumirira kuwakonda.
3 Ndipo anali nao akazi mazana asanu ndi awiri, ana akazi a mafumu, ndi akazi acabe mazana atatu; ndipo akazi ace anapambutsa mtima wace.
4 Ndipo kunali, atakalamba Solomo, akazi ace anapambutsa mtima wace atsate milungu yina; ndipo mtima wace sunakhala wangwiro ndi Yehova Mulungu wace monga mtima wa Davide atate wace.
5 Tsono Solomo anatsata Asitoreti fano la anthu a Zidoni, ndi Milikomu fano lonyansitsa la Aamoni.
6 Ndipo Solomo anacita coipa pamaso pa Yehova, osatsata Yehova ndi mtima wonse monga Davide atate wace.
7 Pamenepo Salomo anamangira Kemosi fano lonyansitsa la Amoabu ndi Moleki fano lonyansitsa la ana a Amoni misanje, pa phiri liri patsogolo pa Yerusalemu.
8 Ndipo momwemo anacitiranso akazi ace onse acilendo, amene amafukizira naphera nsembe mafano ao.
9 Ndipo Yehova anakwiya ndi Solomo, pokhala mtima wace unapambuka kwa Yehova Mulungu wa Israyeli, amene adamuonekera kawiri,
10 namlamulira za cinthu comweci, kuti asatsate milungu yina; koma iye sanasunga cimene Yehova anacilamula.
11 Cifukwa cace Yehova ananena ndi Solomo, Popeza cinthu ici cacitika ndi iwe, ndipo sunasunga cipangano canga ndi malemba anga amene ndinakulamulira, zedi, ndidzakung'ambira ufumu ndi kuupatsa mnyamata wako.
12 Koma m'masiku ako sindidzatero cifukwa ca Davide atate wako, koma ndidzaung'ambira m'manja mwa mwana wako;
13 komatu sindidzacotsa ufumu wonsewo; pfuko limodzi ndidzapatsa mwana wako, cifukwa ca Davide mtumiki wanga, ndi cifukwa ca Yerusalemu amene ndinamsankha.
14 Ndipo Yehova anamuutsira Solomo mdani, ndiye Hadadi M-edomu; iyeyo anali wa mbumba ya mfumu ya ku Edomu.
15 Pakuti pamene Davide adali m'Edomu, ndipo Yoabu kazembe wa nkhondo adanka kukaika akufawo, atapha amuna onse m'Edomu;
16 pakuti Yoabu ndi Aisrayeli onse anakhalako miyezi isanu ndi umodzi, mpaka atawapha amuna onse m'Edomu;
17 Hadadi uja anathawa, iyeyo ndi a ku Edomu ena, akapolo a atate wace pamodzi naye, kumka ku Aigupto, Hadadiyo akali mwana.
18 Ndipo anacoka ku Midyani nafika ku Parani, natenga anthu a ku Parani pamodzi nao, nafika ku Aigupto kwa Farao mfumu ya Aigupto, ameneyo anampatsa nyumba, namnenera zakudya, nampatsako dziko.
19 Ndipo Farao anamkomera mtima ndithu Hadadiyo, nampatsa mkazi ndiye mbale wa mkazi wace, mbale wace wa Takipenesi mkazi wamkulu wa mfumu.
20 Ndipo mbale wa Takipenesi anamuonera Genubati mwana wace, ameneyo Takipenesi anamletsera kuyamwa m'nyumba ya Farao, ndipo Genubati anakhala m'banja la Farao pamodzi ndi ana amuna a Farao.
21 Ndipo atamva Hadadi ku Aigupto kuti Davide anagona ndi makolo ace, ndi kuti Yoabu kazembe wa nkhondo adafanso, Hadadi ananena ndi Farao, Mundilole ndimuke ku dziko la kwathu.
22 Tsono Farao anati kwa iye, Koma cikusowa iwe nciani kwa ine, kuti ufuna kumuka ku dziko la kwanu? Nayankha iye, Palibe kanthu, koma mundilole ndimuke ndithu.
23 Ndipo Mulungu anamuutsira mdani wina, ndiye Rezoni mwana wa Eliyada, amene adathawa mbuye wace Hadadezeri mfumu ya ku Zoba.
24 Iye nasonkhanitsa anthu, nakhala kazembe wa nkhondo, muja Davide anawapha a ku Zobawo, napita ku Damasiko, hakhala komweko, nakhala mfumu ya ku Damasiko.
25 Ndipo iye anali mdani wa Israyeli masiku onse a Solomo, kuonjezerapo coipa anacicita Hadadi, naipidwa nao Aisrayeli, nakhala mfumu ya ku Aramu.
26 Ndipo Yerobiamu mwana wa Nebati M-efrati wa ku Zereda mnyamata wa Solomo, dzina la amace ndiye Zeruwa, mkazi wamasiye, iyenso anakweza dzanja lace pa mfumu.
27 Ndipo cifukwa cakukweza iye dzanja lace pa mfumu ndi cimeneci: Solomo anamanga Milo, namanganso pogumuka pa linga la mudzi wa Davide atate wace.
28 Ndipo munthu ameneyo Yerobiamu anali ngwazi; ndipo pamene Solomo anamuona mnyamatayo kuti ngwacangu, anamuika akhale woyang'anira wa nchito yonse ya nyumba ya Yosefe.
29 Ndipo kunali nthawi yomweyo kuti Yerobiamu anaturuka m'Yerusalemu, ndipo mneneri Ahiya wa ku Silo anampeza m'njira; tsono iyeyo anabvaliratu cobvala catsopano, ndipo iwo awiri anali okha kuthengo.
30 Ndipo Ahiyayo anagwira cobvala cace catsopano, nacing'amba khumi ndi pawiri.
31 Nati kwa Yerobiamu, Takwaya magawo khumi; popeza atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Taona ndidzaung'amba ufumu m'dzanja la Solomo ndi kukupatsa iwe mafuko khumi.
32 Koma iye adzakhala nalo pfuko limodzi, cifukwa ca Davide mtumiki wanga, ndi ca Yerusalemu, mudzi umene ndinausankha m'mafuko onse a Israyeli.
33 Nditero popeza iwo anandisiya, napembedza Asitoreti mulungu wa Azidoni, ndi Kemosi mulungu wa Amoabu, ndi Milikomu mulungu wa ana a Amoni, osayenda m'njira zanga, kucita cimene ciyenera pamaso panga, ndi kusunga malemba anga ndi maweruzo anga, monga umo anatero Davide atate wace.
34 Koma sindidzalanda ufumu wonse m'dzanja lace, koma ndidzamkhalitsa mfumu masiku ace onse, cifukwa ca Davide mtumiki wanga amene uja ndinamsankha, cifukwa kuti anasunga malamulo anga ndi malemba anga.
35 Koma ndidzalanda ufumu m'dzanja la mwana wace, ndi kupatsa iwe mafuko khumi amene.
36 Ndipo ndidzamninkha mwana wace pfuko limodzi, kuti Davide mtumiki wanga akhale cikhalire ndi nyali pamaso panga m'Yerusalemu, mudzi umene ndinadzisankhira kuikapo dzina langa.
37 Ndipo ndidzakutenga iwe, ndipo udzacita ufumu monga umo ukhumbira moyo wako, nudzakhala mfumu ya Israyeli.
38 Ndipo kudzakhala kuti ukadzamvera iwe zonse ndikulamulirazo, nukadzayenda m'njira zanga ndi kucita cilungamo pamaso panga, kusunga malemba anga ndi malamulo anga, monga anatero Davide mtumiki wanga pamenepo Ine ndidzakhala ndi iwe, ndidzakumangira ndi kukukhazikitsira nyumba, monga nelinammangira Davide, ndipo ndidzakupatsa iwe Israyeli.
39 Ndipo cifukwa ca ici nelidzazunza mbumba ya Davide, koma si masiku onse ai.
40 Cifukwa cace Solomo anafuna kupha Yerobiamu, ndipo Yerobiamu anathawira ku Aigupto kwa Sisaki mfumu ya Aigupto, nakhala m'Aigupto kufikira imfa ya Solomo.
41 Ndipo macitidwe otsiriza a Solomo, ndi nchito zace zonse anazicita, ndi nzeru zace, kodi sizilembedwa zimenezo m'buku la madtidwe a Solomo?
42 Ndipo masiku amene Solomo anakhala mfumu ya Aisrayeli onse m'Yerusalemu anali zaka makumi anai.
43 Ndipo Solomo anagona ndi makolo ace, naikidwa m'mudzi wa Davide atate wace; ndipo Rehabiamu mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.
1 Ndipo Rehabiamu anamka ku Sekemu, popeza Aisrayeli onse anadza ku Sekemu kumlonga ufumu.
2 Ndipo kunali kuti Yerobiamu mwana wa Nebati anacimva akali m'Aigupto, kumene anathawira kucokera ku maso a Solomo mfumu, pakuti Yerobiamu anakhala ku Aigupto.
3 Ndipo anatuma akukamuitana. Ndipo Yerobiamu ndi msonkhano wonse wa Israyeli anadza, nalankhulana ndi Rehabiamu, nati,
4 Atate wa nu analemeretsa gori lathu, ndipo inu tsono pepuzaniko nchito zosautsa za atate wanu, ndi gori lolemera lace limene anatisenza, ndipo tidzakutumikirani.
5 Ndipo iye anati kwa iwo, Bamukani, mukagone masiku atatu, pamenepo mukabwera kwa ine. Ndipo anthu anamuka.
6 Ndipo mfumu Rehabiamu anafunsira kwa mandoda, amene anaimirira pamaso pa Solomo atate wace, akali moyoiyeyo, nati, Inu mundipangire bwanji kuti ndiyankhe anthu awa?
7 Ndipo iwo anamuuza kuti, Mukakhala inu mtumiki wa anthu awa lero, ndi kuwatumikira ndi kuwayankha ndi kukamba nao mau okoma, tsono iwo adzakhala cikhalire atumiki anu.
8 Koma iye analeka uphungu wa mandodawo, umene anampangirawo, nakafunsira kwa acinyamata anzace oimirira pamaso pace,
9 nati kwa lwo, Kodi inu mundipangire bwanji kuti tiyankhe anthu awa anandiuza ine, kuti, Mupepuze gori limene atate wanu anatisenza ife?
10 Ndipo acinyamata anzace ananena naye, Dati, Mzitero ndi anthu awa adalankhula nanu, nati, Atate wanu analemeretsa gori lathu, koma inu mutipepuzire limenelo; mzitero nao, Kanense wanga adzaposa m'cuuno mwa atate wanga.
11 Ndipo tsopano, popeza atate wanga anakusenzani gori lolemera, ine ndidzaonjezerapo pa gori lanu, atate wanga anakukwapulani ndi zikoti, koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.
12 Ndipo Yerobiamu ndi anthu onse anabwera kwa Rehabiamu tsiku lacitatu monga momwe anawauzira mfumu, nati, Bweraninso kwa ine tsiku lacitatu.
13 Ndipo mfumu inayankha anthu mau okalipa, naleka uphungu anampangira mandodawo,
14 nalankhula nao monga mwa uphungu wa acinyamata, nati, Atate wanga analemeretsa gori lanu, koma ine ndidzaonjezerapo pa gori lanu; atate wanga anakukwapulani ndi zikoti, koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira,
15 Potero mfumu siinamvera anthuwo, pakuti kusintha uku kunacokera kwa Yehova, kuti akhazikitse mau ace amene Yehova ananenetsa Abiya wa ku Silo kwa Yerobiamu mwana wa Nebati.
16 Ndipo pakuona Aisrayeli onse kuti mfumu siinawamvera iwo, anthuwo anayankha mfumu, Tiri naye ciani Davide? inde tiribe colowa m'mwana wa Jese; tiyeni kwathu Aisrayeli inu; yang'aniranitu, nyumba yako, Davide. Momwemo Aisrayeli anacoka kumka ku mahema ao.
17 Kama ana aja a Israyeli akukhala m'midzi ya Yuda, Rehabiamu anakhalabe mfumu yao.
18 Pamenepo mfumu Rehabiamu anatuma Adoramu wamsonkho, ndipo Aisrayeli onse anamponya miyala, nafa. Ndipo mfumu Rehabiamu anafulumira kulowa m'gareta wace kuthawira ku Yerusalemu.
19 Motero Aisrayeli anapandukana ndi nyumba ya Davide kufikira lero.
20 Ndipo kunali, atamva Aisrayeli onse kuti Yerobiamu wabweranso, anatuma kumuitanira iye kumsonkhano, namlonga iye mfumu ya Aisrayeli onse; palibe munthu anatsata nyumba ya Davide koma pfuko lokha la Yuda.
21 Ndipo Rehabiamu anafika ku Yerusalemu, nasonkhanitsa nyumba yonse ya Yuda, ndi pfuko la Benjamini, ankhondo osankhika zikwi zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu, kuyambana nayo nyumba ya Israyeli, kubwezanso ufumu kwa Rehabiamu mwana wa Solomo.
22 Ndipo mau a Mulungu anafika kwa Semaya mneneri wa Mulungu, nati,
23 Lankhula kwa Rehabiamu mwana wa Solomo mfumu ya Yuda, ndi kwa nyumba yonse ya Yuda, ndi Benjamini, ndi kwa anthu otsalawo, nuti,
24 Yehova atero, Musamuka, ndipo musakayambana ndi abale anu ana a Israyeli, bwererani yense kunyumba kwace; popeza cinthuci cacokera kwa Ine. Ndipo iwo anamvera mau a Yehova, natembenuka, nabwerera monga mwa mau a Yehova.
25 Ndipo Yerobiamu anamanga Sekemu m'mapiri a Efraimu, nakhalamo, naturukamo, namanga Penueli.
26 Ndipo Yerobiamu ananena m'mtima mwace, Ufumuwu udzabwereranso ku nyumba ya Davide.
27 Anthu awa akamakwera kukapereka nsembe m'nyumba ya Yehova m'Yerusalemu, pamenepo mitima ya anthu awa idzatembenukiranso kwa mbuye wao, kwa Rehabiamu mfumu ya Yuda; ndipo adzandipha, nadzabweranso kwa Rehabiamu mfumu ya Yuda.
28 Potero mfumu inakhala upo, napanga ana a ng'ombe awiri agolidi, nati kwa iwo, Kukulemetsani kukwera ku Yerusalemu; tapenyani Aisrayeli inu milungu yanu imene inakuturutsani m'dziko la Aigupto.
29 Ndipo anaimika mmodzi ku Beteli, naimika wina ku Dani.
30 Koma cinthu ici cinasanduka: chimo, ndipo anthu anamka ku mmodziyo wa ku Dani.
31 Iye namanga nyumba za m'misanje, nalonga anthu acabe akhale ansembe, osati ana a Levi ai.
32 Ndipo Yerobiamu anaika madyerero mwezi wacisanu ndi citatu, tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi olingana ndi madyerero aja a ku Yuda, napereka nsembe pa guwa la nsembe; anatero m'Beteli, nawaphera nsembe ana a ng'ombe aja anawapanga, naika m'Beteli ansembe a misanje imene anaimanga.
33 Ndipo anapereka nsembe pa guwa la nsembe analimanga m'Beteli, tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi wacisanu ndi citatu, m'mwezi umene anaulingirira m'mtima mwa iye yekha, nawaikira ana a Israyeli madyerero, napereka nsembe pa guwa la nsembe, nafukiza zonunkhira.
1 Ndipo onani, munthu wa Mulungu anacokera ku Yuda mwa mau a Yehova nadza ku Beteli; ndipo Yerobiamu anali kuimirira m'mbali mwa guwa la nsembe kufukiza zonunkhira.
2 Ndipo iye anapfuula mwa mau a Yehova kutemberera guwa la nsembe, nati, Guwa la nsembe, guwa la nsembe, atero Yehova, Taona mwana adzabadwa m'nyumba ya Davide, dzina lace ndi Yosiya, adzaphera pa iwe ngati nsembe anthu ansembe a misanje, amene alikufukiza zonunkhira pa iwe, nadzatentha pa iwe mafupa a anthu.
3 Ndipo iye anapatsa cizindikilo tsiku lomwelo, nari, Cizindikilo cimene Yehova ananena ndi ici, Taonani guwali la nsembe lidzang'ambika, ndi phulusa liri pa ilo lidzatayika.
4 Ndipo kunacitika, pa kumva mfumu mau a munthu wa Mulungu amene anawapfuula, kutemberera guwa la nsembe m'Beteli, Yerobiamu anatansa dzanja lace ali ku guwalo, nati, Mgwireni iye. Ndipo dzanja lace analitansira kwa iye linauma, kuti sanatha kulipfunyatitsanso.
5 Ndiponso guwalo linang'ambika, ndi phulusa la pa guwalo linatayika, monga mwa cizindikilo cimene munthu wa Mulungu anapatsa mwa mau a Mulungu.
6 Ndipo mfumu inayankha niti kwa munthu wa Mulungu, Undipembedzere Yehova Mulungu wako, nundipempherere, kuti dzanja langa libwerenso kwa ine. Ndipo munthuyo wa Mulungu anapembedza Yehova, ndipo dzanja la mfumu linabwezedwa kwa iye momwemo mwa kale.
7 Mfumu niti kwa munthu wa Mulungu, Tiye kwathu, ukapumule, ndikupatse mphatso.
8 Ndipo munthu wa Mulungu ananena ndi mfumu, Mungakhale mundigawira pakati ndi pakati nyumba yanu, sindilowa kwa inu, kapena kudya mkate, kapena kumwa madzi kuno.
9 Pakuti potero ndinalamulidwa ndi mau a Yehova, ndi kuti, Usakadye mkate, kapena kumwa madzi, kapena kubwerera njira yomweyo unadzerayo.
10 Tsono iye anayenda njira yina osabwerera njira yomweyo anaidzera pakudza ku Beteli.
11 Ndipo ku Beteli kunakhala mneneri wokalamba, ndipo mwana wace wina anadzamfotokozera macitidwe onse anawacita munthu wa Mulunguyo tsiku lomwelo m'Beteli ndi mau ace anawanena ndi mfumu; inde omwe aja iwo anamfotokozera atate wao.
12 Ndipo atate wao anati kwa iwo, Wapitira njira yiti? popeza ana ace adaona njira analowera munthu wa Mulungu anacokera ku Yudayo.
13 Nanena ndi ana ace, Ndimangireni mbereko pa buru. Namangira iwo mbereko pa buru, naberekekapo iye.
14 Natsata munthu wa Mulungu, nampeza ali, tsonga patsinde pa mtengo wathundu, nanena naye, Kodi ndiwe munthu wa Mulungu amene uja anacokera ku Yuda? Nati, Ndine amene.
15 Tsono ananena naye, Tiye kwathu, ukadye mkate.
16 Nan iye, Sindingabwerere nawe kukalowa kwanu, kapena kudya mkate, kapena kumwa nawe madzi pano;
17 pakuti mau a Yehova anadza kwa ine, nati Usakadye mkate, kapena kumwa madzi kumeneko, kapena kubwerera njira yomweyo unadzerayo.
18 Ndipo anati kwa iye, Inenso ndine mneneri wonga iwe, ndipo mthenga analankhula ndi ine mwa mau a Yehova, nati, Kambwezere kwanu, kuti akadye mkate, namwe madzi. Koma anamnamiza.
19 Tsono anabwerera naye, nakadya kwao, namwa madzi.
20 Ndipo kunacitika iwo ali cikhalire pagome, mau a Yehova anadza kwa mneneri amene anambwezayo,
21 napfuula iye kwa munthu uja wa Mulungu anacokera ku Yudayo, nati, Atero Yehova, Pokhala sunamvera mau a pakamwa pa Yehova, osasunga lamulo lija Yehova Mulungu wako anakulamulira,
22 koma unabwerera nudya mkate, ndi kumwa madzi paja pomwe iye anakuuza, Usakadye mkate, kapena kumwa madzi, mtembo wako tsono sudzaikidwa ku manda a atate ako.
23 Ndipo kunacitika, atadya iye mkate, ndi kumwa madzi, anammangira mbereko pa buru mneneri amene anambwezayo.
24 Ndipo atacoka iye, mkango unakomana naye panjira, numupha, ndipo mtembo wace unagwera m'njiramo, buru naima pafupi, mkangonso unaima pafupi ndi mtembo.
25 Ndipo onani, anthu anapitapo naona mtembo wogwera m'njiramo, ndi mkango uli ciimire pafupi ndi mtembo, nadzanena m'mudzi m'mene munakhala mneneri wokalamba uja.
26 Ndipo mneneri amene uja anambweza panjirayo atamva, anati, Ndiye munthu uja wa Mulungu amene sanamvera mau a Yehova; cifukwa cace Yehova wampereka kwa mkango, numkadzula numupha, monga mwa mau a Yehova analankhula nayewo.
27 Iye nanena ndi ana ace, nati, Ndimangireni mbereko pa buru. Namangira mbereko.
28 Namuka iye, napeza mtembo wace wogwera m'njira, ndi buru ndi mkango ziti ciimire pafupi ndi mtembo. Mkango udalibe kudya mtembo, kapena kukadzula buru.
29 Ndipo mneneri ananvamula mtembo wa munthu wa Mulunguyo, nausenza pa buru, nabwera nao, nalowa m'mudzi mneneri wokalamba kumlira ndi kumuika.
30 Ndipo mtembo wace anauika m'manda a iye mwini, namlira iwo maliro, nati, Mayo, mbale wanga!
31 Ndipo kunacitika, atamuika iye, ananena ndi ana ace, nati, Nkadzamwalira ine mudzandiike ine m'manda momwemo mwaikidwa munthu wa Mulunguyo, ikani mafupa anga pafupi ndi mafupa ace.
32 Popeza mau aja anawapfuula mwa mau a Yehova kutemberera guwa la nsembe la ku Beteli, ndi kutemberera nyumba zonse za misanje iri m'midzi ya ku Samariya, adzacitika ndithu.
33 Pambuyo pa ici Yerobiamu sanabwerera pa njira yace yoipa, koma analonganso anthu acabe akhale ansembe a misanje, yensewakufuna yemweyu anampatula akhale wansembe wa misanje,
34 Ndimo umu munali chimo la nyumba ya Yerobiamu, limene linaidula ndi kuiononga pa dziko lapansi.
1 Nthawi yomweyo Abiya mwana wa Yerobiamu anadwala.
2 Ndipo Yerobiamu ananena ndi mkazi wace, Unyamuke, nudzizimbaitse, ungadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yerobiamu, nupite ku Silo; taona, kumeneko kuli Ahiya mneneri uja anandiuza ine ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
3 Nupite nayo mikate khumi, ndi timitanda, ndi cigulu ca uci, numuke kwa iye; adzakuuza m'mene umo akhalire mwanayo.
4 Natero mkazi wa Yerobiamu, nanyamuka namka ku Silo, nalowa m'nyumba ya Ahiya. Koma Ahiya sanatha kupenya, popeza maso ace anali tong'o, cifukwa ca ukalamba wace.
5 Ndipo Yehova ananena ndi Ahiya, Taona, mkazi wa Yerobiamu akudza kukufunsa za mwana wace, popeza adwala; udzanena naye mwakuti mwakuti; popeza kudzakhala pakulowa iye adzadzizimbaitsa.
6 Ndipo kunacitika, pamene Ahiya anamva mgugu wa mapazi ace alinkulowa pakhomo, anati, Lowa mkazi iwe wa Yerobiamu, wadzizimbaitsiranji? pakuti ine ndatumidwa kwa iwe ndi mau olasa.
7 Kauze Yerobiamu, Atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Ndingakhale ndinakukulitsa pakati pa anthu, ndi kukukhalitsa mfumu ya anthu anga Aisrayeli,
8 ndipo ndinalanda nyumba ya Davide ufumu, ndi kuupereka kwa iwe, koma sunafanana ndi Davide mtumiki wanga uja, amene anasunga malamulo anga, nanditsata ndi mtima wace wonse kucita zolunjika zokha zokha pamaso panga;
9 koma wacimwa koposa onse akale, nukadzipangira milungu yina ndi mafano yoyenga kundikwiyitsa, nunditaya Ine kumbuyo kwako;
10 cifukwa cace, taona, ndidzafikitsa coipa pa nyumba ya Yerobiamu, ndi kugurula mwana wamwamuna yense wa Yerobiamu womangika ndi womasuka m'Israyeli, ndipo ndidzacotsa psiti nyumba yonse ya Yerobiamu, monga munthu acotsa ndowe kufikira idatha yonse.
11 Agaru adzadya ali yense wa Yerobiamu wakufa m'mudzi; ndi mbalame za m'mlengalenga zidzadya yense wakufera kuthengo; popeza wanena ndi Yehova.
12 Tanyamuka tsono, numuke kwanu; pakulowa mapazi ako m'mudzi mwanayo adzatsirizika.
13 Ndipo Aisrayeli onse adzamlira, nadzamuika, popeza iye yekha wa ana a Yerobiamu adzalowa m'manda; pakuti mwa iye mwapezedwa cokoma ca kwa Yehova Mulungu wa Israyeli m'nyumba ya Yerobiamu.
14 Ndiponso Yehova adzadziukitsira mfumu ya Israyeli, idzaononga nyumba ya Yerobiamu tsiku lomwelo; nciani ngakhale tsopano apa?
15 Popeza Yehova adzawakantha Aisrayeli monga bango ligwedezeka ndi madzi, nadzazula Aisrayeli m'dziko lino labwino analipatsa makolo ao, nadzawamwazira ku tsidya lija la Firate, popeza iwo anapanga zifanizo zao zokwiyitsa Yehova.
16 Ndipo adzai pereka Aisrayeli cifukwa ca macimo a Yerobiamu anacimwawo, nacimwitsa nao Aisrayeli.
17 Ndipo mkazi wa Yerobiamu ananyamuka nacoka, nafika ku Tiriza; ndipo polowa iye pa khomo la nyumba yace anatsirizika mwanayo.
18 Ndipo anamuika, namlira Aisrayeli, monga mwa mau a Yehova anawalankhula pa dzanja la mtumiki wace Ahiya mneneri.
19 Ndipo macitidwe ena a Yerobiamu m'mene umo anacitira nkhondo, ndi m'mene umo anacitira ufumu, taona, analembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli.
20 Ndipo masiku akukhala Yerobiamu mfumu anali zaka makumi awiri mphambu ziwiri, nagona iye kwa makolo ace, nalowa ufumu m'malo mwace Nadabu mwana wace.
21 Ndipo Rehabiamu mwana wa Solomo anali mfumu ya dziko la Yuda. Rehabiamu anali wa zaka makumi anai mphambu cimodzi polowa ufumu wace, nakhala mfumu zaka khumi mphambu zisanu ndi ziwiri m'Yerusalemu, m'mudzi m'mene Yehova adausankha m'mafuko onse a Israyeli kukhazikamo dzina lace. Ndipo dzina la amace linali Naama M-amoni.
22 Ndipo Ayuda anacita zoipa pamaso pa Yehova, namcititsa nsanje ndi zoipa zao anazicitazo, zakuposa zija adazicita makolo ao,
23 Pakuti anadzimangiranso misanje, ndi zoimiritsa, ndi zifanizo, pa citunda conse cacitali, ndi patsinde pa mtengo wogudira uli wonse;
24 panalinso anyamata ocitirana dama m'dzikomo; iwo amacita monga mwa zonyansitsa za amitundu, amene Yehova anapitikitsa pamaso pa ana a Israyeli.
25 Ndipo kunacitika, Rebabiamu atakhala mfumu zaka zisanu, Sisaki mfumu ya Aigupto anakwera ndi nkhondo ku Yerusalemu,
26 nacotsa cuma ca m'nyumba ya Yehova, ndi cuma ca m'nyumba ya mfumu; inde anacotsa conseco, nacotsanso zikopa zagolidi zonse adazipanga Solomo.
27 Ndipo mfumu Rehabiamu anapanga m'malo mwa izo zikopa zina zamkuwa, nazipereka m'manja a akapitao a olindirira, akusunga pakhomo pa nyumba ya mfumu.
28 Ndipo kunacitika, pakulowa mfumu m'nyumba ya Yehova, olindirira aja anazinyamula, nabweranso nazo ku cipinda ca olindirirawo.
29 Tsono, macitidwe ace ena a Rehabiamu, ndi zonse anazicita, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?
30 Ndipo panali nkhondo pakati pa Rehabiamu ndi Yerobiamu masiku ao onse.
31 Nagona Rehabiamu ndi makolo ace, naikidwa kwa makolo ace m'mudzi wa Davide. Ndipo dzina la amace linali Naama M-amoni, nalowa ufumu m'malo mwace Abiya mwana wace.
1 Ndipo caka cakhumi mphambu zisanu ndi zitatu ca mfumu Yerobiamu mwana wa Nebati, Abiya analowa ufumu wa Yuda.
2 Anakhala mfumu zaka zitatu m'Yerusalemu, ndipo dzina la amace linali Maaka mwana wa Abisalomu.
3 Nayenda iye m'zoipa zonse za atate wace, zimene iye adacita asanalowe ufumu Abiyayo; ndipo mtima wace sunali wangwiro ndi Yehova Mulungu wace monga mtima wa Davide kholo lace.
4 Koma cifukwa ca Davideyo Yehova Mulungu wace anampatsa nyali m'Yerusalemu, kumuikira mwana wace pambuyo pace, ndi kukhazikitsa Yerusalemu;
5 cifukwa kuti Davide adacita colungama pamaso pa Yehova, osapambuka masiku ace onse pa zinthu zonse adamlamulira iye, koma cokhaco cija ca Uriya Mhiti.
6 Ndipo panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yerobiamu masiku onse a moyo wace.
7 Ndipo macitidwe ace ena a Abiya, ndi zonse anazicita, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda? Ndipo panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yerobiamu.
8 Nagona Abiya ndi makolo ace, namuika anthu m'mudzi wa Davide; Asa mwana wace nalowa ufumu m'malo mwace.
9 Ndipo caka ca makumi awiri ca Yerobiamu mfumu ya Israyeli, Asa anayamba kukhala mfumu ya Yuda.
10 Nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi anai mphambu cimodzi, ndipo dzina la amace linali Maaka mwana wa Abisalomu.
11 Ndipo Asa anacita zabwino pamaso pa Yehova monga Davide kholo lace.
12 Nacotsa m'dziko anyamata aja adama, nacotsanso mafano onse anawapanga atate ace.
13 Ndipo anamcotsera Maaka amace ulemu wa mace wa mfumu, popeza iye anapanga fano lonyansitsa likhale cifanizo; ndipo Asa analikha fano lace, nalitentha ku mtsinje wa Kidroni.
14 Koma misanje sanaicotsa, koma mtima wa Asa unali wangwiro ndi Yehova masiku ace onse.
15 Ndipo analonga m'nyumba ya Yehova zinthu zija atate wace adazipereka; napereka zinthu zina iye mwini zasiliva ndi zagolidi ndi zotengera.
16 Ndipo panali nkhondo pakati pa Asa ndi Basa mfumu ya Israyeli masiku ao onse.
17 Ndipo Basa mfumu ya Israyeli anakwera ndi nkhondo ku Yuda, namanga ku Rama kuwaletsa anthu asaturuke kapena kulowa kwa Asa mfumu ya Yuda.
18 Tsono Asa anatenga siliva yense ndi golidi yense anatsala pa cuma ca nyumba ya Yehova, ndi cuma ciri m'nyumba ya mfumu, nazipereka m'manja mwa anyamata ace; ndipo mfumu Asa anazitumiza kwa Benihadadi mwana wa Tabrimoni, mwana wa Hezroni mfumu ya Aramu, wakukhala ku Damasiko, nati,
19 Pakhale pangano pakati pa ine ndi inu, pakati pa atate wanga ndi atate wanu; taonani, ndatumiza kwa inu mphatso ya siliva ndi golidi, tiyeni lilekeke pangano liri pakati pa inu ndi Basa mfumu ya Israyeli, kuti andicokere.
20 Ndipo Benihadadi anamvera mfumu Asa, natuma akazembe a nkhondo ace kukathira nkhondo ku midzi ya Israyeli, napasula Iyoni, ndi Dani, ndi AbeliBeti-Maaka, ndi Kineroti wonse, ndi dziko lonse la Nafitali.
21 Tsono Basa atamva izi, analeka kumanga ku Rama nakhala pa Tiriza.
22 Pamenepo mfumu Asa anamemeza Ayuda onse, osatsala ndi mmodzi yense; natuta miyala ya ku Rama, ndi mitengo yomwe, akamange nayo Basa; ndi mfumu Asa anamangira Geba wa ku Benjamini, ndi Mizipa.
23 Ndipo macitidwe onse ena a Asa, ndi mphamvu yace yonse, ndi zonse anazicita, ndi midzi anaimanga, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda? Koma masiku a ukalamba wace anadwala mapazi ace.
24 Nagona Asa ndi makolo ace, naikidwa kwa makolo ace m'mudzi wa Davide kholo lace; ndipo Yosafati mwana wace analowa ufumu m'malo mwace.
25 Ndipo Nadabu mwana wa Yerobiamu analowa ufumu wa Israyeli caka caciwiri ca Asa mfumu ya Yuda, nakhala mfumu ya Israyeli zaka ziwiri.
26 Nacita zoipa pamaso pa Yehova, nayenda m'njira ya atate wace, ndi m'chimo lomwelo iye akacimwitsa nalo Aisrayeli.
27 Ndipo Basa mwana wa Akiya, wa nyumba ya Isakara, anampangira ciwembu; ndipo Basa anamkanthira ku Gibetoni wa Afilisti, popeza Nadabu ndi Aisrayeli onse adamangira misasa Gibetoni.
28 Inde Basa anamupha caka cacitatu ca Asa mfumu ya Yuda, nalowa ufumu m'malo mwace.
29 Tsonokunacitika, pokhalamfumu iye, anakantha nyumba yonse ya Yerobiamu, osasiyako wamoyo ndi mmodzi yense wa Yerobiamu, kufikira adamuononga monga mwa mau a Yehova, amene analankhula pa dzanja la mtumiki wace Ahiya wa ku Silo;
30 cifukwa ca macimo a Yerobiamu, amene adacimwa nao, nacimwitsa nao Aisrayeli, ndi kuutsa kwace kumene anaputa nako mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israyeli.
31 Ndipo macitidwe ena a Nadabu, ndi zonse anazicita, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?
32 Ndipo panali nkhondo pakati pa Asa ndi Basa mfumu ya Israyeli masiku ao onse.
33 Tsono Basa mwana wa Ahiya analowa ufumu wa Israyeli caka cacitatu ca Asa mfumu ya Yuda, nakhala mfumu ku Tiriza zaka makomi awiri mphambu zinai.
34 Ndipo anacimwa pamaso pa Yehova, nayenda m'njira ya Yerobiamu, ndi m'chimo lace iye anacimwitsa nalo Israyeli.
1 Ndipo mau a Yehova akutsutsa Basa anadza kwa Yehu mwana wa Hanani, nati,
2 Popeza ndinakukuza iwe kucokera kupfumbi, ndi kukuika iwe mfumu ya anthu anga Israyeli, koma iwe unayenda m'njira ya Yerobiamu, ndi kucimwitsa anthu anga Israyeli, kuputa mkwiyo wanga ndi macimo ao;
3 taona, ndidzacotsa psiti Basa ndi nyumba yace, ndipo ndidzafanizitsa nyumba yako ndi nyumba ya Yerobiamu mwana wa Nebati,
4 Agaru adzadya ali yense wa Basa amene adzafera m'mudzi, ndipo amene adzafera m'thengo zidzamudya mbalame za m'mlengalenga.
5 Tsono macitidwe ena a Basa, ndi nchito zace, ndi mphamvu zace, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?
6 Nagona Basa ndi makolo ace, naikidwa ku Tiriza; ndipo Ela mwana wace analowa ufumu m'malo mwace.
7 Ndiponso mau a Yehova anadza ndi dzanja la mneneri Yehu mwana wa Hanani, kutsutsa Basa ndi nyumba yace, cifukwa ca zoipa zonse anazicita iye pamaso pa Yehova; popeza anaputa mkwiyo wace ndi macitidwe a manja ace, nafanana ndi nyumba ya Yerobiamu; ndiponso popeza anaikantha.
8 Ndipo caka ca makumi awiri mphambu zisanu ndi cimodzi ca Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Basa analowa ufumu wa Israyeli ku Tiriza, nakhala mfumu zaka ziwiri.
9 Ndipo mnyamata wace Zimri, ndiye woyang'anira dera lina la magareta ace, anampangira ciwembu; koma iye anali m'Tiriza kumwa ndi kuledzera m'nyumba ya Ariza, ndiye woyang'anira nyumba m'Tiriza.
10 Nalowamo Zimri, namkantha, namupha caka ca makomi awiri mphambu zisanu ndi ziwiri ca Asa mfumu ya Yuda, nalowa ufumu m'malo mwace.
11 Ndipo kunali, atalowa ufumu wace, nakhala pa mpando wacifumu wace, anawakantha onse a m'nyumba ya Basa, osamsiyira mwana wamwamuna ndi mmodzi yense, kapena wa abale ace, kapena wa mabwenzi ace.
12 Motero Zimri anaononga nyumba yonse ya Basa, monga mwa mau a Yehova, amene ananena akumtsutsa Basa, mwa dzanja la Yehu mneneri,
13 cifukwa ca macimo onse a Basa, ndi macimo a Ela mwana wace anacimwawo, nacimwitsa nao Aisrayeli, kuputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israyeli ndi zacabe zao.
14 Tsono macitidwe ena a Ela, ndi nchito zace zonse, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?
15 Ndipo caka ca makumi awiri mphambu zisanu ndi ziwiri ca Asa mfumu ya Yuda, Zimri anali mfumu masiku asanu ndi awiri ku Tiriza. Ndipo anthu analikumangira misasa Gibetoni wa Afilisti.
16 Koma anthu aja omangira misasa anamva kuti Zimri wacita ciwembu, nakanthanso mfumu; cifukwa cace tsiku lomwelo Aisrayeli onse a kumisasa anamlonga Omri kazembe wa nkhondo akhale mfumu ya Israyeli.
17 Ndipo Omri anacoka ku Gibetoni, ndi Aisrayeli onse naye, nakamangira misasa Tiriza.
18 Kunali tsono, pakuona Zimri kuti nkhondo yalowa m'mudzi, anakwera pa nsanja ya nyumba ya mfumu, nadzitenthera ndi mota nyumba ya mfumu, nafa;
19 cifukwa ca macimo ace anacimwawo, pakucita coipa pamaso pa Yehova; popeza anayenda m'njira ya Yerobiamu, ndi m'chimo lace anacimwa nalolo, nacimwitsa nalo Aisrayeli.
20 Macitidwe ena tsono a Zimri, ndi ciwembu anacicitaco, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?
21 Pamenepo anthu a Israyeli anagawika pakati, anthu ena anatsata Tibini mwana wa Ginati kumlonga ufumu, ena natsata Omri.
22 Koma anthu akutsata Omri anapambana iwo akutsata Tibini mwana wa Ginati; nafa Tibini, Omri nakhala mfumu.
23 Caka ca makumi atatu ndi cimodzi ca Asa mfumu ya Yuda, Omri anayamba kukhala mfumu ya Israyeli, nakhala zaka khumi ndi ziwiri; ku Tiriza anali mfumu zaka zisanu ndi cimodzi.
24 Ndipo anagula kwa Semeri citunda ca Samaria ndi matalente awiri a siliva, namanga pacitundapo, nacha dzina lace la mudzi anaumanga Samaria, monga mwa dzina la Semeri mwini citundaco.
25 Koma Omri anacimwa pamaso pa Yehova, nacita zoipa koposa onse adamtsogolerawo.
26 Nayenda m'njira yonse ya Yerobiamu mwana wa Nebati, ndi chimo lace anacimwitsa nalo Aisrayeli, kuputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israyeli ndi zacabe zao.
27 Ndipo macitidwe ena a Omri anawacita, ndi mphamvu yace anaionetsa, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?
28 Nagona Omri ndi makolo ace, naikidwa m'Samaria; ndipo Ahabu mwana wace analowa ufumu m'malo mwace.
29 Ndipo caka ca makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu ca Asa mfumu ya Yuda Ahabu mwana wa Omri analowa ufumu wa Israyeli, nakhala Ahabu mwana wa Omri mfumu ya Israyeli m'Samaria zaka makumi awiri mphambu ziwiri.
30 Ndipo Ahabu mwana wa Omri anacimwa pamaso pa Yehova koposa onse adamtsogolerawo.
31 Ndipo kunali monga ngati kunamcepera kuyenda m'macimo a Yerobiamu mwana wa Nebati, iye anakwatira Yezebeli mwana wamkazi wa Etibaala mfumu ya Azidoni, natumikira Baala, namgwadira,
32 Nammangira Baala guwa la nsembe m'nyumba ya Baala anaimanga m'Samaria.
33 Ahabu anapanganso cifanizo; ndipo Ahabu amene anapambana mafumu onse a Israyeli adamtsogolerawo, kuputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israyeli,
34 M'masiku ace Hiyeli wa ku Beteli anamanga Yeriko; pokhazika maziko ace anadzifetsera Abiramu mwana wace woyamba, poimika zitseko zace anadzifetsera Zegubi mwana wace wotsiriza; monga mwa mau a Yehova amene ananenetsa Yoswa mwana wa Nuni.
1 Ndipo Eliya wa ku Tisibe wokhala ku Gileadi ananena ndi Ahabu, nati, Pali Yehova Mulungu wa Israyeli, amene ndimakhala pamaso pace, ngati adzagwa mame kapena mvula zaka izi, koma ntanena ine ndipo.
2 Ndipo mau a Yehova anadza kwa iye, nati,
3 Coka kuno, nutembenukire kum'mawa, ukabisale kumtsinje Keriti uli ku Yordano.
4 Ndipo kudzakhala kuti uzikamwa mumtsinje, ndipo ndalamulira makungubwi kukudyetsa kumeneko.
5 Momwemo iye anamuka, nacita monga mwa mau a Yehova, nakakhala kumtsinje Keriti uli ku Yordano.
6 Ndipo makungubwi anamtengera mkate ndi nyama m'mawa, ndi mkate ndi nyama madzulo; namamwa iye mumtsinje.
7 Ndipo kunacitika, atapita masiku ena mtsinje udaphwa, popeza munalibe mvula m'dziko.
8 Ndipo mau a Yehova anadza kwa iye, nati,
9 Nyamuka, pita ku Zarefati wa ku Zidoni, nukhale kumeneko; taona, ndamlamulira mkazi wamasiye wa kumeneko akudyetse.
10 Tsono iye ananyamuka namka ku Zarefati, nafika ku cipata ca mudzi; ndipo taona mkazi wamasiye anali kutola nkhuni; ndipo iye anamuitana, nati, Unditengere madzi pang'ono m'cikho, ndimwe.
11 Ndipo m'mene analikumuka kukatenga iye anamuitananso, nati, Unditengerenso kanthongo ka mkate m'dzanja lako.
12 Nati iye, Pali Yehova Mulungu wako, ndiribe mkate, koma kaufa dzanja limodzi kali m'mbiya, ndi mafuta pang'ono m'nsupa; ndipo taona, ndirikutola nkhuni ziwiri kuti ndikadziphikire odekha ndi mwana wanga, tidye, tife.
13 Ndipo Eliya anati kwa iye, Usacita mantha, kacite monga umo wanenamo, koma thanga wandiocerako kamkate, nubwere nako kwa ine; ndipo utatero udziphikire wekha ndi mwana wako.
14 Popeza atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Mbiya ya ufa siidzatha, ndipo nsupa ya mafuta siidzacepa, kufikira tsiku lakugwetsa mvula Yehova pa dziko lapansi.
15 Ndipo iye anakacita monga mwa mau a Eliya, nadya iye mwini, ndi iyeyo, ndi a m'nyumba ace, masiku ambiri.
16 Mbiya ya ufa siidatha, ndi nsupa ya mafuta siinacepa, monga mwa mau a Yehova amene ananenetsa Eliya.
17 Ndipo kunali, zitatha izi, mwana wa mkazi mwini nyumbayo anadwala; ndipo pokula nthenda yace, analeka kupuma.
18 Ndipo mkaziyo ananena ndi Eliya, Ndiri nawe ciani munthu iwe wa Mulungu? Kodi wadza kwa ine kundikumbutsa chimo langa, ndi kundiphera mwana wanga?
19 Ndipo ananena naye, Ndipatse mwana wako. Namtenga m'mfukato mwace napita naye ku cipinda cosanja cogonamo iyeyo; namgoneka pa kama wa iye mwini.
20 Napfuulira kwa Yehova, nati, Yehova Mulungu wanga, kodi mwamgwetsera coipa mkazi wamasiye amene ndikhala naye, kumphera mwanace?
21 Nafungatira katatu pa mwanayo, napfuulira kwa Yehova, nati, Yehova Mulungu wanga, ndikupemphanf, ubwere moyo wace wa mwanayu m'cifuwa mwace.
22 Ndipo Yehova anamvamau a Eliya, ndipo moyo wa mwanayo unalowanso mwa iye, nakhalanso moyo.
23 Ndipo Eliya ananyamula mwanayo, natsika naye ku cipinda cosanja, nalowa naye m'nyumba, nampereka kwa amace; nati Eliya, Taona, mwana wako ali moyo.
24 Ndipo mkazi anati kwa Eliya, Ndizindikira tsopano kuti ndinu munthu wa Mulungu, ndi kuti mau a Yehova ali m'kamwa mwanuwo ngoona.
1 Ndipo atapita masiku ambiri, mau a Yehova anafika kwa Eliya caka cacitatu, nati, Kadzionetse kwa Ahabu, ndipo ndidzatumiza mvula padziko.
2 Ndipo Eliya anamka kukadzionetsa kwa Ahabu. Ndipo njala inali yaikuru m'Samaria.
3 Ndipo Ahabu anaitana Obadiya woyang'anira nyumba yace. Koma Obadiya anaopa ndithu Yehova;
4 pakuti pamene Yezebeli anapulula aneneri a Yehova, Obadiya anatenga aneneri zana limodzi, nawabisa makumi asanu asanu m'phanga, nawadyetsa mkate ndi madzi.
5 Ndipo Ahabu anati kwa Obadiya, Kayendere dziko lonse ku zitsime zonse zamadzi, ndi ku mitsinje yonse, kapena tikapeza msipu ndi kusunga moyo wa akavalo ndi nyuru, zingafe nyama zonse.
6 Tsono iwo awiri anagawana dziko kukaliyendera; Ahabu anadzera njira yace yekha, ndi Obadiya njira yina yekha.
7 Ndipo Obadiya ali m'njira, taona, Eliya anakomana naye; iye namdziwa, namgwadira, nati, Ndinu kodi mbuye wanga Eliya?
8 Ndipo anamyankha, nati, Ndine amene; kauze mbuye wako kuti Eliya wabwera,
9 Iye nati, Ndacimwanji kuti mupereka kapolo wanu m'dzanja la Ahabu kundipha?
10 Pali Yehova Mulungu wanu, ngati kuli mtundu umodzi wa anthu, kapena ufumu, kumene mbuye wanga sanatumako kukufunani, ndipo pakunena iwo, Palibe iye, analumbiritsa ufumu umene ndi mtundu umene kuti sanakupezani.
11 Ndipo tsopano mukuti, Kauze mbuye wako kuti Eliya wabwera.
12 Ndipo kudzacitika, ine ntakusiyani, mzimu wa Yehova udzakunyamulirani kosakudziwa ine, ndipo ine ntakauza Ahabu, ndipo akalephera kukupezani, adzandipha. Koma ine kapolo wanu ndimaopa Yehova kuyambira ubwana wanga.
13 Kodi sanakuuzani mbuye wanga cimene ndidacita m'kuwapha Yezebeli aneneri a Yehova, kuti ine ndidabisa aneneri a Yehova zana limodzi makumi asanu asanu m'phanga, ndikuwadyetsa mkate ndi madzi?
14 Ndipo tsopano inu mukuti, Kauze mbuye wako Eliya wabwera, ndipo adzandipha.
15 Koma Eliya anati, Pali Yehova wa makamu, amene ndikhala pamaso pace, zedi, ndionekadi pamaso pace lero.
16 Ndipo Obadiya anauka kukomana ndi Ahabu, namuuza, ndipo Ahabu ananka kukomana ndi Eliya.
17 Ndipo kunacitika pamene Ahabu anaona Eliya, Ahabu anati kwa iye Kodi ndiwe uja umbvuta Israyeliyo?
18 Nati iye, Sindimabvuta Israyeli ine ai, koma inu ndi nyumba ya atate wanu; popeza munasiya malamulo a Yehova, ndi kutsata Abaala.
19 Ndipo tsono, tumani mundimemezere Aisrayeli onse ku phiri la Karimeli, ndi aneneri a Baala mazana anai mphambu makumi asanu, ndi aneneri a cifanizoco mazana anai, akudya pa gome la Yezebeli.
20 Pamenepo Ahabu anatumiza mau kwa ana onse a Israyeli, namemeza aneneri onse ku phiri la Karimeli.
21 Ndipo Eliya anayandikira kwa anthu onse, nati, Mukayika-kayika kufikira liti? ngati Yehova ndiye Mulungu, mtsateni iye; ngati Baala, mumtsate iyeyo. Ndipo anthu nnena kumyankha mau amodzi.
22 Ndipo Eliya ananena ndi anthuwo, Ine ndatsala ndekha mneneri wa Yehova, koma aneneri a Baala ndiwo anthu mazana anai mphambu makumi asanu.
23 Atipatse tsono ng'ombe ziwiri; ndipo adzisankhire iwo eni ng'ombe imodzi, naiduledule, naiike pankhuni osasonkhapo moto; ndipo ine ndidzakonza ng'ombe yinayo, ndi kulika pankhuni osasonkhapo moto.
24 Ndipo muitane inu dzina la mulungu wanu, ine ndidzaitana dzina la Yehova; ndipo Mulunguyo ayankhe ndi mote ndiye Mulungu. Ndipo anthu onse anabvomera, nati, Ndiwo mau abwino amene.
25 Pamenepo Eliya ananena ndi aneneri a Paala, Dzisankhireni ng'ombe imodzi yanu, muyambe kuikonza, popeza mucuruka; nimuitane dzina la mulungu wanu, koma musasonkhepo moto.
26 Ndipo iwo anatenga ng'ombe ija adawapatsa, naikonza, naitana dzina la Baala, kuyambira m'mawa kufikira pausana, nati, Baala, timvereni ife. Koma panalibe mau kapena wobvomereza. Ndipo anabvinabvina kuguwa adalimanga.
27 Ndipo pausana Eliya anawaseka, nati, Kwezani mau, popeza ndiye mulungu; kapena alikulingirira, kapena wapambuka, kapena ali paulendo, kaya agona, adzagalamuka.
28 Ndipo anakwezadi mau, nadzitema monga makhalidwe ao ndi mipeni ndi nthungo, kuti mwazi wao unali cucucu.
29 Ndipo kunali, litapendeka dzuwa, ananenera kufikira nthawi ya kupereka nsembe; koma panalibe mau, kapena wobvomereza, kapena wakuwamvera.
30 Pamenepo Eliya ananena ndi anthu onse, Senderani kwa ine; ndipo onse anasendera kwa iye. Iye nakonza guwa la nsembe la Yehova lidagumukalo.
31 Ndipo Eliya anatenga miyala khumi ndi iwiri, monga mwa ciwerengo ca mafuko a ana a Yakobo, amene mau a Yehova adamfikira, kuti, Dzina lako ndi Israyeli.
32 Ndipo ndi miyalayi anamanga guwa la nsembe m'dzina la Yehova, nazunguniza guwalo ndi mcera, ukulu wace ngati kulandira miyeso iwiri ya mbeu kuzinga guwalo.
33 Ndipo anakonza nkhunizo, naduladula ng'ombe, naiika pankhuni. Nati, Dzazani madzi mbiya zinai, muwathire pa nsembe yopsereza ndi pankhuni.
34 Nati, Bwerezaninso kawiri; nabwerezanso. Nati, Bwerezani katatu; nabwereza katatu.
35 Ndipo madzi anayenda pozinga guwa la nsembe, nadzazanso meerawo ndi madzi.
36 Ndipo kunali, nthawi ya kupereka nsembe yamadzulo, Eliya mneneri anasendera, nati, Yehova Mulungu wa Abrahamu ndi Isake ndi Israyeli, lero kudziwike kuti Inu ndinu Mulungu wa Israyeli, ndi ine mtumiki wanu, kuti mwa mau anu ndacita zonsezi.
37 Ndimvereni Yehova, ndimvereni, kuti anthu awa adziwe kuti Inu Yehova ndinu Mulungu, ndi kuti Inu mwabwezanso mitima yao.
38 Pamenepo moto wa Yehova unagwa, nutentha nsembe yopsereza, ndi nkhuni, ndi miyala, ndi pfumbi, numwereretsa madzi anali mumcera.
39 Ndipo anthu onse anaona, nagwa nkhope zao pansi, nati, Yehova ndiye Mulungu, Yehova ndiye Mulungu.
40 Ndipo Eliya anati kwa iwo, Gwirani aneneri a Baala, asapulumuke ndi mmodzi yense. Nawagwira, ndipo Eliya ana pita nao ku mtsinje wa Kisoni, nawapha pamenepo.
41 Ndipo Eliya ananena ndi Ahabu, Nyamukani, idyani, imwani; popeza kumveka mkokomo: wa mvula yambiri.
42 Ndipo Ahabu anakadya, namwa; koma Eliya anakwera pamwamba pa Karimeli, nagwadira pansi, naika nkhope yace pakati pa maondo ace.
43 Ndipo anati kwa mnyamata wace, Kwera kapenyerere kunyanja. Iye nakwera, napenyetsetsa, nati, Kulibe kanthu. Nati, Bwerezanso kasanu ndi kawiri.
44 Ndipo kunali kacisanu ndi ciwiri anati, Taonani, kwaturuka kunyanja kamtambo konga dzanja la munthu. Nati iye, Kauze Ahabu, kuti, Mangani gareta, tsikani, mvula Ingakutsekerezeni.
45 Ndipo kunali, polinda kanthawi, thambo linada ndi mitambo ndi mphepo, nigwa mvula yaikuru. Ndipo Ahabu anayenda m'gareta, namuka ku Yezreeli.
46 Ndipo dzanja la Yehova tinakhala pa Eliya; namanga iye za m'cuuno mwace, nathamanga m'tsogolo mwa Ahabu ku cipata ca Yezreeli.
1 Ndipo Ahabu anauza Yezebeli zonse anazicita Eliya, ndi m'mene anawaphera ndi lupanga aneneri onsewo,
2 Tsono Yezebeli anatuma mthenga kwa Eliya, wakuti, Milungu indilange nionjezepo, ngati sindilinganiza moyo wako ndi moyo wa mmodzi wa iwowo mawa nthawi yomwe yino.
3 Ndipo iye ataona cimeneci, ananyamuka, nathawa kupulumutsa moyo, nafika ku Beereseba wa ku Yuda, nasiya mnyamata wace pamenepo.
4 Koma iye mwini analowa m'cipululu ulendo wa tsiku limodzi, nakakhala pansi patsinde pa mtengo watsanya, napempha kuti afe; nati, Kwafikira, cotsani tsopano moyo wanga, Yehova; popeza sindiri wokoma woposa makolo anga.
5 Ndipo anagona tulo patsinde pa mtengo watsanya; ndipo taonani, wamthenga anamkhudza, nati kwa iye, Uka nudye.
6 Ndipo anaceuka, naona kumutu kunali kamkate kooca pamakala, ndi mkhate wa madzi. Tsono anadya namwa, nagonanso pansi,
7 Ndipo mthenga wa Yehova anafikanso kaciwiri, namkhudza, nati, Tauka, idya, popeza ulendo udzakulaka.
8 Tsono anauka, nadya namwa, nayenda ndi mphamvuya cakudya cimeneco masiku makumi anai usana ndi usiku, nafika ku phiri la Mulungu ku Horebu.
9 Nafika kuphanga, nagona kumeneko, ndipo taonani, mau a Yehova anamfikira, nati kwa iye, Ucitanji pano, Eliya?
10 Ndipo anati, Ine ndinacitira cangu Yehova Mulungu wa makamu; popeza ana a Israyeli anasiya cipangano canu, napasula maguwa anu a nsembe, napha aneneri anu ndi lupanga, ndipo ndatsala ndekha, ndipo afuna moyo wanga kuucotsa.
11 Ndipo iye anati, Turuka, nuime pa phiri tino pamaso pa Yehova. Ndipo taonani, Yehova anapitapo, ndi mphepo yaikuru ndi yamphamvu inang'amba mapiri, niphwanya matanthwe pamaso pa Yehova; koma Yehova sanakhala m'mphepomo. Itapita mphepoyo kunali cibvomezi; komanso Yehova sanali m'cibvomezico.
12 Citaleka cibvomezi panali moto; koma Yehova sanali m'motomo, Utaleka mota panali bata la kamphepo kayaziyazi.
13 Ndipo atamva Eliya, anapfunda nkhope yace ndi copfunda cace, naturuka, naima pa khomo la phangalo. Ndipo taonani, anamdzera mau akunena naye, Ucitanji kuno, Eliya?
14 Nati iye, Ndacitira cangu Yehova Mulungu wa makamu; popeza ana a Israyeli ataya cipangano canu, nagumula maguwa a nsembe anu, napha aneneri anu ndi lupanga; ndipo ndatsala ndekha, ndipo afuna moyo wanga kuucotsa.
15 Ndipo Yehova anati kwa iye, Bwerera ulendo wako, udzere kucipululu kumka ku Damasiko, ndipo utafikako udzoze Hazaeli akhale mfumu ya Aramu;
16 ukadzozenso Yehu mwana wa Nimsi akhale mfumu ya Israyeli; ukadzozenso Elisa mwana wa Safati wa ku Abelimehola akhale mneneri m'malo mwako.
17 Ndipo kudzacitika Yehu adzamupha amene adzapulumuka ku lupanga la Hazaeli; ndi Elisa adzamupha amene adzapulumuka ku lupanga la Yehu,
18 Ndiponso ndidasiya m'lsrayeli anthu zikwi zisanu ndi ziwiri osagwadira Baala maondo ao, osampso-mpsona ndi milomo yao.
19 Tsono anacokako, napeza Elisa mwana wa Safati alikukoketsa cikhasu ng'ombe ziwiri ziwiri magori khumi ndi awiri, iye yekha anakhala pa gori lakhumi ndi ciwiri; ndipo Eliya anamka kunali iyeyo, naponya copfunda cace pa iye.
20 Ndipo iye anasiya ng'ombe zija, namthamangira Eliya, nati, Ndiloleni ndithange ndakapsompsona atate wanga ndi amai wanga; nditatero ndidzakutsatani. Nati iye, Bwerera, ndakucitanji?
21 Ndipo anabwerera panali iye uja, natengako ng'ombe ziwiri, nazipha, naphikira nyama yace ndi zipangizo za zocitira nazo ng'ombe, napatsa anthu adye. Atatero, ananyamuka, natsata Eliya, namtumikira.
1 Ndipo Benihadadi mfumu ya Aramu anamemeza khamu lace lonse la nkhondo; ndi mafumu makumi atatu mphambu awiri anali naye, pamodzi ndi akavalo ndi magareta; nakamangira Samaria misasa, naponyana nao nkhondo.
2 Natumiza mithenga lrumudzi kwa Ahabu mfumu ya Israyeli, nati kwa iye,
3 Atero Benihadadi, Siliva wako ndi golidi wako ndi wanga, akazi ako ndi ana ako omwe okometsetsawo ndi anga.
4 Ndipo mfumu ya Israyeli anayankha, nati, Monga mwanena, mbuye wanga mfumu, ndine wanu ndi zonse ndiri nazo.
5 Tsono mithenga ija inabwerera, niti, Atero Benihadadi, kuti, Ndinatumadi kwa iwe, ndi kuti, Uzindipatsa siliva wako, ndi golidi wako, ndi akazi ako, ndi ana ako;
6 koma mawa dzuwa lino ndidzatuma anyamata anga kwa iwe, nadzafunafuna m'nyumba mwako, ndi m'nyumba za anyamata ako; ndipo kudzakhala kuti cifuniro conse ca maso ako adzacigwira ndi manja ao, nadzacicotsa.
7 Pamenepo mfumu ya Israyeli anaitana akulu onse a dziko, nati, Tazindikirani inu, penyani kuti-munthu uyu akhumba coipa; popeza anatuma kwa ine kulanda akazi anga, ndi ana anga, ndi siliva, ndi golidi wanga; ndipo sindinamkaniza.
8 Ndipo akulu onse ndi anthu onse anati kwa iye, Musamvere, musabvomereze.
9 Ndipo anati kwa mithenga ya Benihadadi, Kauzeni mbuye wanga mfumu, Zonse munayamba kundituma mtumiki wanu kuzifunsa ndidzacita, koma ici sindingacicite. Nicoka mithengayo, nimbwezera mau.
10 Ndipo Benihadadi anatuma kwa iye, nati, Milungu indilange, nionjezepo, ngati pfumbi la Samaria lidzafikira kudzaza manja a anthu onse akutsata mapazi anga.
11 Ndipo mfumu ya Israyeli anayankha, nati, Kamuuzeni, Wakumanga zida asadzikuze ngati wakubvulayo.
12 Ndipo kunacitika, atamva Benihadadi mau awa, analikumwa nao mafumu m'misasa, ananena ndi anyamata ace, Nikani. Nandandalika pamudzipo.
13 Ndipo taonani, mneneri anadza kwa Ahabu mfumu ya Israyeli, nati, Atero Yehova, Kodi waona unyinji uwu waukuru wonse? Taonani, ndidzaupereka m'dzanja mwako lero, kuti udziwe kuti ndine Yehova.
14 Nati Ahabu, Mwa yam? Nati, Atero Yehova, Mwa anyamata a akalonga a madera. Natinso, Adzayamba kuponya nkhondo ndani? Nati, Iwe.
15 Pamenepo anawerenga anyamata a akalonga a madera, nawapeza mazana awiri mphambu makumi atatu kudza awiri. Pamenepo anawerenganso anthu onse, ndiwo ana a Israyeli onse zikwi zisanu ndi ziwiri.
16 Ndipo amenewo anaturuka usana. Koma Benihadadi analinkumwa naledzera m'misasamo, iye ndi mafumu aja makumi atatu mphambu awiri aja akumthandiza.
17 Ndipo anyamata a akalonga a madera anayamba kuturuka, koma Benihadadi anatuma anthu, iwo nambwezera mau, kuti, M'Samaria mwaturuka anthu.
18 Nati iye, Cinkana aturukira mumtendere, agwireni amoyo; cinkana aturukira m'nkhondo, agwireni amoyo.
19 Tsono anaturuka m'mudzi anyamata a akalonga a madera aja, ndi khamu la nkhondo linawatsata.
20 Ndipo ali yense anapha munthu wace; ndipo Aaramu anathawa, Aisrayeli nawapitikitsa; ndipo Benihadadi mfumu ya Aramu anathawira pa kavalo pamodzi ndi apakavalo.
21 Tsono mfumu ya Israyeli inaturuka, nikantha apakavalo ndi apamagareta, nawapha Aaramuwo maphedwe akuru.
22 Ndipo mneneri uja anayandikira kwa mfumu ya Israyeli, nati kwa iye, Kadzilimbitseni, mudziwe mucenjere ndi cimene mucicita; popeza caka cikudzaci mfumu ya Aramu idzabweranso kulimbana nanu.
23 Ndipo anyamata a mfumu ya Aramu anati kwa iye, Milungu yao nja kumapiri, ndimo m'mene atilakira; koma tikaponyana nao kucidikha, zedi tidzaposa mphamvu.
24 Tsono citani ici, cotsani mafumu aja yense ku malo ace, muike m'malo mwao akazembe.
25 Ndipo mudziwerengere khamu la nkhondo longa khamu lija lidaonongekalo, ndi akavalo onga akavalo aja, ndi magareta monga omwe aja; ndipo tikaponyane nao pacidikha tidzawapambana ndithu. Namvera iye mau ao, natero kumene.
26 Tsono kunacitika, pakufikanso caka Benihadadi anamemeza Aaramu nakwera ku Meld kukaponyana ndi Aisrayeli.
27 Ndipo Aisrayeli anamemezananso, anali naye kamba, nakakomana nao; ndipo Aisrayeli anamanga misasa yao pandunji pao, ngati timagulu tiwiri ta ana a mbuzi; koma Aaramu anadzaza dziko.
28 Ndipo munthu uja wa Mulungu anafikako, nalankhula ndi mfumu ya Israyeli, nati, Atero: Yehova, Popeza Aaramu amati, Yehova ndiye Mulungu wa kumapiri, osati Mulungu wa kuzigwa, mwa ici ndidzapereka unyinji uwu waukuru m'dzanja mwako, kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova.
29 Ndipo awa anakhala m'misasa pandunji pa ajawo masiku asanu ndi awiri. Tsono kunali, tsiku lacisanu ndi ciwiri anayambana nkhondo; ndipo ana a Israyeli anaphako Aaramu tsiku limodzi anthu oyenda pansi zikwi zana limodzi.
30 Ndipo otsalawo anathawira ku Afeki kumudzi, ndipo linga linawagwera anthu zikwi makumi awiri mphambu asanu ndi awiri amene adatsalawo. Ndipo Benihadadi anathawa, nalowa m'mudzi, m'cipinda ca m'katimo.
31 Pamenepo anyamata ace anati kwa iye, Taonani, tidamva ife kuti mafumu a nyumba ya Israyeli ndi mafumu acifundo; tiyeni tibvale ciguduli m'cuuno mwathu, ndi zingwe pamitu pathu, titurukire kwa mfumu ya Israyeli, kapena adzakusungirani moyo.
32 Motero anabvala ciguduli m'cuuno mwao, ndi zingwe pamitu pao, nafika kwa mfumu ya Israyeli, nati, Kapolo wanu Benihadadi ati, Ndiloleni ndikhale ndi moyo. Nati iye, Akali moyo kodi? Ndiye mbale wanga.
33 Tsono anthuwo anamyang'anitsa, nafulumira kugwira mauwo ngati anaterodi; nati, Mbale wanu Benihadadi ali moyo, Nati, Kamtengeni, Pamenepo Benihadadi anaturuka, nadza kwa iye, ndipo iye anamkweza m'gareta mwaceo
34 Ndipo Benihadadi anati kwa iye, Ndidzabweza midzi ija atate wanga analanda kwa atate wanu; ndipo mudzikonzere mabwalo a malonda m'Damasiko, monga umo atate wanga anadzikonzera m'Samaria. Ndi ine, ati Ahabu, ndikulola umuke ndi pangano ili. Tsono anapangana naye, namlola amuke.
35 Ndipo wina wa ana a aneneri ananena ndi mnzace mwa mau a Yehova, Undikanthe ine, Koma munthuyo anakana kumkantha.
36 Ndipo ananena naye, Popeza sunamvera mau a Yehova, taona, utalekana nane mkango udzakupha, Ndipo m'mene atalekana naye, mkango unampeza, numupha.
37 Ndipo amene uja anakomana ndi munthu wina, nati, Undikanthe. Namkantha munthuyu, namtema pomkantha.
38 Pamenepo mneneriyo anamuka, nadikira mfumu pamseu, nadzizimbaitsa ndi mpango pamaso pace.
39 Ndipo popitapa mfumu, anapfuula kwa mfumu, nati, Kapolo wanu analowa pakati pa nkhondo, ndipo taonani, munthu anapambuka nabwera ndi munthu kwa ine, nati, Tasunga munthu uyu; akasowa ndi cifukwa ciri conse moyo wako udzakhala m'malo mwa moyo wace, kapena udzalipa talenti la siliva.
40 Tsono pocita kapolo wanu apo ndi apo ndapeza palibe. Ndipo mfumu ya Israyeli inati kwa iye, Mlandu wako ukutsutsa momwemo, wadziweruza wekha.
41 Ndipo iye anafulumira kucotsa mpango kumaso kwace, ndi mfumu ya Israyeli inaona kuti anali mmodzi wa aneneri.
42 Niti kwa iye, Atero Yehova, Popeza wataya m'dzanja lako munthu uja ndinati ndimuononge konse, moyo wako udzakhala m'malo mwamoyo wace, ndi anthu ako m'malo mwa anthu ace.
43 Pamenepo mfumu ya Israyeli inamka kwao wamsunamo ndi wokwiya, nafika ku Samaria.
1 Ndipo zitatha izi, kunaoneka zotere: Naboti wa ku Yezreeli anali ndi munda wamphesa, unali m'Yezreelimo, m'mbali mwa nyumba ya Ahabu mfumu ya ku Samaria.
2 Ndipo Ahabu analankhula ndi Naboti, nati, diloleni Ndipatse munda wako wamphesa ukhale munda wanga wa ndiwo, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga; ndipo m'malo mwace ndidzakupatsa munda wamphesa wokoma woposa uwu; kapena kukakukomera ndidzakupatsa ndalama za pa mtengo wace,
3 Ndipo Naboti anati kwa Ahabu, Pali Yehova, ndi pang'ono ponse ai, kuti ndikupatseni colowa ca makolo anga,
4 Ndipo Ahabu analowa m'nyumba mwace wamsunamo ndi wokwiya, cifukwa ca mau amene Naboti wa ku Yezreeli adalankhula naye; popeza adati, Sindikupatsani colowa ca makolo anga. M'mwemo anagona pa kama wace, nayang'ana kumbali, nakana kudya mkate.
5 Koma Yezebeli mkazi wace anadza kwa iye, nati kwa iye, Mucitiranji msunamo, kuti mukana kudya mkate?
6 Nati kwa iye, Popeza ndinalankhula kwa Naboti wa ku Yezreeli, ndinati kwa iye, Undigulitse munda wako ndi ndalama; kapena ukafuna, ndikupatsa munda wina m'malo mwace; kama anandiyankha, Sindikupatsani munda wanga wamphesa.
7 Ndipo Yezebeli mkazi wace anati kwa iye, Kodi mulamulira Aisrayeli tsopano ndinu? Taukani, idyani mkate, ukondwere mtima wanu; munda wa Naboti wa ku Yezreeli ndidzakupatsani ndine.
8 M'mwemo analemba akalata m'dzina la Ahabu nakhomerapo cizindikilo cace, natumiza akalatawo kwa akulu ndi omveka anali m'mudzi mwace, nakhala naye Naboti.
9 Ndipo analemba m'akalata, nati, Lalikirani kuti asale kudya, muike Naboti pooneka ndi anthu;
10 ndipo muike anthu awiri, anthu oipa, pamaso pace, kuti amcitire umboni, ndi kuti, Watemberera Mulungu ndi mfumu; nimumturutse ndi kumponya miyala kumupha.
11 Ndipo anthu aja a mudzi wace, ndiwo akulu ndi omveka adakhala m'mudzi mwace, anacita monga Yezebeli anawatumizira, monga munalembedwa m'akalata amene iye anawatumizira.
12 Analalikira kuti asale kudya, naike Naboti pooneka ndi anthu.
13 Ndipo anthu aja awiri oipawo analowa, nakhala pamaso pace, ndipo anthu oipawo anamcitira umboni wonama Nabotiyo, pamaso pa anthu onse, nati, Naboti anatemberera Mulungu ndi mfumu. Pamenepo anamturutsa m'mudzi, namponya miyala, namupha.
14 Pomwepo anatuma mau kwa Yezebeli, nati, Naboti waponyedwa miyala, nafa.
15 Ndipo kunali, atamva Yezebeli kuti anamponya Naboti miyala nafa, Yezebeli anati kwa Ahabu, Taukani, landirani munda wamphesa wa Naboti Myezreeli uja anakana kukugulitsani ndi ndarama, popeza, Naboti sali ndi moyo, koma wafa.
16 Ndipo kunali, atamva Ahabu kuti Naboti wafa, Ahabu anauka kukatsikira ku munda wamphesa wa Naboti, kuulandira.
17 Ndipo mau a Yehova anadza kwa Eliya waku Tisibe, nati,
18 Nyamuka, tsikira kukakomana ndi Ahabu mfumu ya Israyeli, akhala m'Samariya; taona, ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene anatsikira kukaulandira.
19 Ndipo uzilankhula naye, ndi kuti, Atero Yehova, Kodi wapha, mulandanso? Nulankhulenso naye, kuti, Atero Yehova, Paja agaru ananyambita mwazi wa Naboti, pompaja agaru adzanyambita mwazi wako, inde wako.
20 Ndipo Ahabu anati kwa Eliya, Wandipeza kodi, mdani wangawe? Nayankha, Ndakupeza; pokhala wadzigulitsa kucita coipaco pamaso pa Yehova.
21 Taona, ndidzakufikitsira coipa, ndi kucotsa mbumba yako psiti; ndipo ndidzalikhira Ahabu mwana wamwamuna yense, ndi yense womangika ndi womasuka m'lsrayeli;
22 ndipo ndidzalinganiza nyumba yako ndi nyumba ya Yerobiamu mwana wa Nebati, ndi ya Basa mwana wa Ahiya; cifukwa ca kuputa kumene unaputa nako mkwiyo wanga, ndi kucimwitsa Israyeli.
23 Ndipo za Yezebeli yemwe Yehova ananena, nati, Agaru adzadya Yezebeli ku linga la Yezreeli.
24 Mwana ali yense wa Ahabu amene adzafera m'mudzi, agaru adzamudya; ndipo iye amene adzafera kuthengo, mbalame za m'mlengalenga zidzamudya,
25 Koma panalibe wina ngati Ahabu wakudzigulitsa kucita coipa pamaso pa Yehova, amene Yezebeli mkazi wace anamfulumiza.
26 Ndipo anacita moipitsitsa kutsata mafano, monga mwa zonse amazicita Aamori, amene Yehova adawapitikitsa pamaso pa ana a Israyeli.
27 Ndipo kunali, pakumva Ahabu mau amenewa, anang'amba zobvala zace, nabvala ciguduli pathupi pace, nasala kudya, nagona paciguduli, nayenda nyang'anyang'a.
28 Pamenepo mau a Yehova anadza kwa Eliya wa ku Tisibe, nati,
29 Waona umo wadzicepetsera Ahabu pamaso panga? Popeza adzicepetsa pamaso panga, sindidzafikitsa coipa cimeneci akali moyo iye; koma m'masiku a mwana wace ndidzacifikitsa pa nyumba yace.
1 Ndipo Aaramu ndi Aisrayeli anakhala cete zaka zitatu, osathirana nkhondo.
2 Koma kunacitika caka cacitatu, kuti Yehosafati mfumu ya Yuda anatsikira kwa mfumu ya Israyeli.
3 Ndipo mfumu ya Israyeli ananena ndi anyamata ace, nati, Kodi simudziwa kuti Ramoti Gileadi ngwathu, ndipo tangokhala cete, osaulanditsa m'dzanja la mfumu ya Aramu.
4 Tsono anati kwa Yehosafati, Kodi udzapita nane kunkhondo ku Ramoti Gileadi? Ndipo Yehosafati anati kwa mfumu ya Israyeli, M'mene ukhalira iwe ndi momwe ndikhalira ndine; anthu anga monga anthu ako, akavalo anga monga akavale ako.
5 Ndipo Yehosafati ananena ndi mfumu ya Israyeli, Fuusira ku mau a Yehova lero.
6 Pamenepo mfumu ya Israyeli inasonkhanitsa aneneri ngati anthu mazana anai, nanena nao, Kodi ndizimuka kukathira nkhondo pa Ramoti Gileadi, kapena ndileke? Nati iwo, Kweraniko; popeza Ambuye adzaupereka m'dzanja la mfumu.
7 Koma Yehosafati anati, Kodi pano palibe mneneri wina wa Yehova, kuti tifunsire kwa iye?
8 Ndipo mfumu ya Israyeli inati kwa Yehosafati, Alipo munthu wina kuti tifunsire kwa Yehova mwa iye; koma ndimuda, popeza samanenera za ine zabwino, koma zoipa; ndiye Mikaya mwana wace wa Yimla. Nati Yehosafati, Isamatero mfumu.
9 Tsono mfumu ya Israyeli anaitana mdindo, nati, Kamtenge msanga Mikaya mwana wa Yimla.
10 Ndipo mfumu ya Israyeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anakhala onse awiri, yense pa mpando wacifumu wace, obvala zobvala zao zacifumu pabwalo pa khomo la cipata ca Samaria; ndipo aneneri onse ananenera pamaso pao.
11 Ndipo Zedekiya mwana wa Kenana anadzisulira nyanga zacitsulo, nati, Atero Yehova, Ndi izi mudzagunda nazo Aaramu mpaka atatha psiti,
12 Ndipo aneneri onse ananena momwemo, nati, Kwerani ku Ramoti Gileadi, ndipo mudzacita mwai; popeza Yehova adzaupereka m'dzanja la mfumu.
13 Tsono mthenga uja udakaitana Mikaya unanena naye, nati, Taona, mau a aneneri abvomerezana zokoma kwa mfumu ndi m'kamwa m'modzi; mau ako tsono afanane ndi mau a wina wa iwowo, nunene zabwino.
14 Koma Mikaya anati, Pali Yehova, zimene Yehova adzanena nane ndidzanena ine.
15 Ndipo atafika kwa mfumu, mfumu inati kwa iye, Mikaya, kodi tizimuka ku Ramoti Gileadi kukathira nkhondo, kapena tileke? Nati iye, Kwerani, ndipo mudzacita mwai, popeza Yehova adzaupereka m'dzanja la mfumu.
16 Ndipo mfumu inati, Ndikulumbiritse kangati kuti undiuze zoona zokha zokha m'dzina la Yehova?
17 Nati iye, Ndinaona Aisrayeli onse obalalika pamapiri ngati nkhosa zopanda mbusa; ndipo Yehova anati, Izi ziribe mwini, yense abwerere ndi mtendere ku nyumba yace.
18 Pamenepo mfumu ya Israyeli inanena ndi Yehosafati, Kodi sindinakuuza kuti uyu sadzanenera za ine zabwino, koma zoipa?
19 Ndipo anati, Cifukwa cace tamverani mau a Yehova, Ndinaona Yehova alikukhala pa mpando wace wacifumu, ndi khamu lonse la Kumwamba liri ciriri m'mbali mwace, ku dzanja lamanja ndi lamanzere,
20 Nati Yehova, Adzanyenga Ahabu ndani, kuti akwere nagwe ku Ramoti Gileadi? Ndipo anati wina mwakuti, wina mwakuti.
21 Pamenepo mzimu wina unaturuka, nuima pamaso pa Yehova, nuti, Ndidzamnyenga ndine. Nati Yehova kwa iye, Motani?
22 Nati, Ndidzaturuka, ndidzakhala mzimu wonama m'kamwa mwa aneneri ace onse. Nati, Udzamnyengadi, nudzakhozanso; turuka, ukatero kumene.
23 Ndipo tsopano taonani, Yehova waika mzimu wonama m'kamwa mwa aneneri anu onse awa, ndipo Yehova ananena coipa ca inu.
24 Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenana anasendera, napanda Mikaya patsaya, nati, Mzimu wa Yehova wandicokera bwanji, kulankhula ndi iwe?
25 Mikaya nati, Taona, udzapenya tsiku lolowa iwe m'cipinda ca pakati kubisala.
26 Pamenepo inati mfumu ya Israyeli, Tengani Mikaya, mumbweze kwa Amoni kalonga wa mudzi, ndi kwa Yoasi mwana wa mfumu;
27 ndipo muziti, Itero mfumu, Khazikani uyu m'kaidi, mumdyetse cakudya ca nsautso, ndi madzi a nsautso, mpaka ndikabwera ndi mtendere.
28 Ndipo Mikaya anati, Mukabwera ndithu ndi mtendere Yehova sanalankhula mwa ine. Nati, Mvetsani, anthu inu nonse.
29 Tsono mfumu ya Israyeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anakwera ku Ramoti Gileadi.
30 Ndipo mfumu ya Israyeli inanena ndi Yehosafati, Ine ndidzadzizimbaitsa, ndi kulawa kunkhondo, koma bvala iwe zobvala zako zacifumu. Ndipo mfumu ya Israyeli inadzizimbaitsa, nilowa kunkhondo.
31 Tsono mfumu ya Aramu idalamulira akapitao makumi atatu mphambu ziwiri za magareta ace, niti, Musaponyana ndi anthu ang'ono kapena akuru, koma ndi mfumu ya Israyeli yokha.
32 Ndipo kunali, akapitao a magareta ataona Yehosafati, anati, Zedi uyu ndiye mfumu ya Israyeli imene, napotolokera kukaponyana naye; koma Yehosafati anapfuula.
33 Ndipo pamene akapitao a magareta anaona kuti sindiye mfumu ya Israyeli, anabwerera osampitikitsa.
34 Ndipo munthu anakoka uta wace ciponyeponye, nalasa mfumu ya Israyeli pakati pa maluma a maraya acitsulo; tsono ananena ndi mnyamata wa gareta wace, Tembenuza dzanja lako, nundicotse kunkhondo, popeza ndalasidwa.
35 Ndipo nkhondo inakula tsiku lomwelo, ndipo mfumu inagwirizidwa m'gareta mwace kupenyana ndi Aaramu, natsirizika madzulo; ndipo mwazi unaturuka m'bala pa phaka la gareta.
36 Ndipo mfuu unafikira khamu lonse la nkhondo polowa dzuwa, ndi kuti, Yense kumudzi kwao, ndi yense ku dziko la kwao.
37 Ndipo inafa mfumu, naifikitsa ku Samaria, naika mfumu m'Samaria.
38 Ndipo potsuka garetayo pa thawale la ku Samaria agaru ananyambita mwazi wace, pala pamasamba akazi adama, monga mwa mau a Yehova amene ananenawo.
39 Tsono macitidwe ena a Ahabu, ndi zonse adazicita, ndi nyumba ya minyanga adaimanga, ndi midzi yonse adaimanga, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?
40 Ndipo Ahabu anagona ndi makolo ace; ndi Ahaziya mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.
41 Koma Yehosafati mwana wa Asa anayamba kukhala mfumu ya Yuda caka cacinai ca Ahabu mfumu ya Israyeli.
42 Yehosafati anali wa zaka makumi atatu mphambu zisanu, pamene analowa ufumu, nakhala nifumu zaka makumi awiri mphambu zisanu m'Yerusalemu. Ndi dzina la amace linali Azuba mwana wa Sili.
43 Ndipo anayenda m'njira yonse ya atate wace Asa, osapambukamo; nacita coyenera pamaso pa Yehova, koma misanje sanaicotsa; anthu anapherabe nsembe, nafukiza zonunkhira pamsanje.
44 Ndipo Yehosafati anacitana mtendere ndi mfumu ya Israyeli.
45 Tsono maciddwe ena a Yehosafati, ndi mphamvu anaionetsayo, ndi umo anathira nkhondo, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?
46 Ndipo anacotsa m'dziko anyamata onyansa aja adatsalira masiku a atate wace Asa.
47 Ndipo m'Edomu munalibe mfumu, koma kazembe wa mfumu.
48 Yehosafati anamanga zombo za ku Tarsisi kukatenga golidi ku Ofiri; koma sizinamuka, popeza zinaphwanyika pa Ezioni Geberi.
49 Pamenepo Ahaziyamwana wa Ahabu ananena ndi Yehosafati, Anyamata anga amuke pamodzi ndi anyamata anu m'zombo. Koma Yehosafati anakana.
50 Ndipo Yehosafati anagona ndi makolo ace, naikidwa ndi makolo ace m'mudzi wa Davide kholo lace; ndipo Yoramu mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.
51 Ahaziya mwana wa Ahabu anayamba kukhala mfumu ya Israyeli pa Samaria m'caka cakhumi mphambu zisanu ndi ziwiri ca Yehosafati mfumu ya Yuda; nakhala mfumu ya Israyeli zaka ziwiri.
52 Nacita coipa pamaso pa Yehova, nayenda m'njira ya atate wace, ndi ya amace, ndi ya Yerobiamu mwana wa Nebati, amene adacimwitsa Israyeli.
53 Natumikira Baala, namweramira, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israyeli, monga umo anacitira atate wace.