1

1 NYIMBO yoposa, ndiyo ya Solomo.

2 Mnyamatayo andipsompsonetse ndi m'kamwa mwace; Pakuti cikondi cako ciposa vinyo.

3 Mafuta ako anunkhira bwino; Dzina lako likunga mafuta onunkhira otsanulidwa; Cifukwa cace anamwali akukonda.

4 Undikoke; tikuthamangire; Mfumu yandilowetsa m'zipinda zace: Tidzasangalala ndi kukondwera ndi iwe. Tidzachula cikondi cako koposa vinyo: Akukonda molungama.

5 Wakuda ine, koma wokongola, Ana akazinu a ku Yerusalemu, Ngati mahema a Kedara, Ngati nsaru zociriga za Solomo.

6 Musayang'ane pa ine, pakuti ndada, Pakuti dzuwa landidetsa. Ana amuna a amai anandikwiyira, Anandisungitsa minda yamipesa; Koma munda wanga wanga wamipesa sindinausunga.

7 Ndiuze, iwe amene moyo wanga ukukonda, Umaweta kuti gulu lako? Umaligonetsa kuti pakati pa usana? Pakuti ndikhalirenji ngati wosocera Pambali pa magulu a anzako?

8 Ngati sudziwa, mkaziwe woposa kukongola, Dzituruka kukalondola bande la gululo, Nukawete ana a mbuzi zako pambali pa mahema a abusa.

9 Ndakulinganiza, wokondedwa wanga mnyamatawe, Ngati akavalo a magareta a Farao.

10 Masaya ako akongola ndi nkhata zatsitsi, Ndi khosi lako ndi zinganga za mkanda wonyezimira.

11 Tidzakupangira nkhata zagolidi Ndi njumu zasiliva.

12 Pokhala mfumu podyera pace, Mphoka yanga inanunkhira.

13 Wokondedwa wanga mnyamatayo ali kwa ine ngati thumba la nipa, Logona pakati pa maere anga.

14 Wokondedwa wanga ali kwa ine ngati cipukutu ca maluwa ofiira M'minda yamipesa ya ku Engedi.

15 Taona, wakongolatu, bwenzi langa; namwaliwe taona, wakongola, Maso ako akunga a nkhunda.

16 Taona, wakongolatu, bwenzi langa, mnyamatawe, inde, wakongoletsa; Pogona pathu mpa msipu.

17 Mitanda ya nyumba zathu nja mikungudza, Ndi mapaso athu nga mlombwa.

2

1 Ndine duwa lofiira la ku Saroni, Ngakhale kakombo wa kuzigwa.

2 Ngati kakombo pakati pa minga Momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana akazi.

3 Ngati maula pakati pa mitengo ya m'nkhalango, Momwemo wokondedwa wanga pakati pa ana amuna. Ndinakondwa pakukhala pa mthunzi wace, Zipatso zace zinatsekemera m'kamwa mwanga.

4 Anandifikitsa ku nyumba ya vinyo, Mbendera yace yondizolimira inali cikondi.

5 Mundilimbikitse ndi mphesa zouma, munditonthoze mtima ndi maula, Pakuti ndadwala ndi cikondi.

6 Dzanja lace lamanzere anditsamiritse kumutu, Dzanja lace lamanja ndi kundifungatira.

7 Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu, Pali mphoyo, ndi nswala za kuthengo, Kuti musautse, ngakhale kugalamutsa cikondi, Mpaka cikafuna mwini.

8 Mau a wokondedwa wanga mnyamatayo! Taona, adza, Alikulumpha pamapiri, alikujidimuka pazitunda.

9 Wokondedwa wanga akunga mphoyo, pena mwana wa mbawala: Taona, aima patseri pa khoma pathu, Apenyera pazenera, Nasuzumira pamade.

10 Wokondedwa wanga analankhula, nati kwa ine, Tauka, bwenzi langa, wokongola wanga, tiye.

11 Pakuti, taona, cisanu catha, Mvula yapita yaleka;

12 Maluwa aoneka pansi; Nthawi yoyimba mbalame yafika, Mau a njiwa namveka m'dziko lathu;

13 Mkuyu uchetsa nkhuyu zace zosakhwima, Mipesa niphuka, Inunkhira bwino. Tauka, bwenzi langa, wokongola wangawe, tiyetu.

14 Nkhunda yangawe, yokhala m'ming'alu ya thanthwe, mobisika motsetsereka, Ndipenye nkhope yako, ndimve manako; Pakuti mau ako ngokoma, nkhope yako ndi kukongola.

15 Mutigwirire ankhandwe, ngakhale ang'ono, amene akuononga minda yamipesa; Pakuti m'minda yathu yamipesa muphuka biriwiri.

16 Wokondedwa wanga ndi wa ine, ine ndine wace: Aweta zace pakati pa akakombo,

17 Mpaka dzuwa litapepa, mithunzi ndi kutanimpha, Bwera, bwenzi langawe, nukhale ngati mphoyo pena mwana wa mbawala Pa mapiri a mipata.

3

1 Usiku pamphasa panga ndinamfunafuna amene moyo wanga umkonda: Ndinamfunafuna, koma osampeza.

2 Ndinati, Ndiuketu, ndiyendeyende m'mudzi, M'makwalala ndi m'mabwalo ace, Ndimfunefune amene moyo wanga umkonda: Ndimfunafuna, koma osampeza.

3 Alonda akuyendayenda m'mudzi anandipeza: Ndinati, Kodi munamuona amene moyo wanga umkonda?

4 Nditawapitirira pang'ono, Ndinampeza amene moyo wanca umkonda: Ndinamgwiriziza, osamfumbatula, Mpaka nditamlowetsa m'nyumba ya amai, Ngakhale m'cipinda ca wondibala.

5 Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu, Pali mphoyo, ndi nswala ya kuthengo, Kuti musautse, ngakhale kugalamutsa cikondi, Mpaka cikafuna mwini.

6 Ndaniyu akwera kuturuka m'cipululu ngati utsi wa tolo, Wonunkhira ndi nipa ndi mtanthanyerere, Ndi zonunkhiritsa zonse za wogulitsa?

7 Taonani, ndi macila a Solomo; Pazingapo amuna amphamvu makumi asanu ndi limodzi, A mwa ngwazi za Israyeli.

8 Onsewo agwira lupanga, nazolowera nkhondo: Yense ali ndi lupanga lace pancafu pace, Cifukwa ca upandu wa usiku.

9 Solomo mfumu anadzipangira macila okhalamo tsonga Ndi matabwa a ku Lebano.

10 Anapanga timilongoti tace ndi siliva, Ca pansi pace ndi golidi, mpando wace ndi nsaru yakuda, Pakati pace panayalidwa za cikondi ca ana akazi a ku Yerusalemu.

11 Turukani, ana akazi inu a Ziyoni, mupenye Solomo mfumu, Ndi korona amace anambveka naye tsiku la ukwati wace, Ngakhale tsiku lakukondwera mtima wace.

4

1 Taona, wakongola, bwenzi langa, namwaliwe, taona, wakongola; Maso ako akunga a nkhunda patseri pa cophimba cako: Tsitsi lako likunga gulu la mbuzi, Zooneka pa phiri la Gileadi.

2 Mano ako akunga gulu la nkhosa zosengasenga, Zokwera kucokera kosamba; Yonse iri ndi ana awiri, Palibe imodzi yopoloza.

3 Milomo yako ikunga mbota yofiira, M'kamwa mwako ndi kukoma: Palitsipa pako pakunga phande la khangaza Patseri pa cophimba cako.

4 Khosi lako likunga nsanja ya Davide anaimangira zida, Apacikapo zikopa zikwi, Ngakhale zikopa zonse za amuna amphamvu,

5 Maere ako awiri akunga ana awiri a nswala obadwa limodzi, Akudya pakati pa akakombo.

6 Mpaka dzuwa litapepa, mithunzi ndi kutanimpha, Ndikamuka ku phiri la nipa, Ndi ku citunda ca mtanthanyerere.

7 Wakongola monse monse, wokondedwa wanga, namwaliwe, Mulibe cirema mwa iwe.

8 Idza nane kucokera ku Lebano, mkwatibwi, Kucokera nane ku Lebano: Unguza pamwamba pa Amana, Pa nsonga ya Seniri ndi Hermoni, Pa ngaka za mikango, Pa mapiri a anyalugwe.

9 Walanda mtima wanga, mlongwanga, mkwatibwi; Walanda mtima wanga ndi diso lako limodzi, Ndi cinganga cimodzi ca pakhosi pako,

10 Ha, cikondi cako ncokongola, mlongwanga, mkwatibwi! Kodi cikondi cako siciposa vinyo? Kununkhira kwa mphoka yako ndi kuposa zonunkhiritsa za mitundu mitundu!

11 M'milomo yako, mkwatibwi, mukukha uci, Uci ndi mkaka ziri pansi pa lilime lako; Kununkhira kwa zobvala zako ndi kunga kununkhira kwa Lebano,

12 Mlongwanga, mkwatibwi ndiye munda wotsekedwa; Ngati kasupe wotsekedwa, ndi citsime copikiza.

13 Mphukira zako ndi munda wamakangaza, Ndi zipatso zofunika, bonongwe ndi mphoka,

14 Mphoka ndi cikasu, Nzimbe ndi ngaho, ndi mitengo yonse yamtanthanyerere; Nipa ndi khonje, ndi zonunkhiritsa zonse zomveka.

15 Ndiwe kasupe wa m'minda, Citsime ca madzi amoyo, Ndi mitsinje yoyenda yocokera ku Lebano.

16 Galamuka, mphepo ya kumpoto iwe, nudze, mphepo iwe ya kumwela; Nuombe pamunda panga, kuti zonunkhiritsa zace ziturukemo. Bwenzi langa mnyamatayo, alowe m'munda mwace, Nadye zipatso zace zofunika.

5

1 Ndalowa m'munda mwanga, mlongwanga, mkwatibwi: Ndachera nipa yanga ndi zonunkhiritsa zanga; Ndadya uci wanga ndi cisa cace; Ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Idyani, atsamwalinu, Imwani, mwetsani cikondi.

2 Ndinagona tulo, koma mtima wanga unali maso: Ndi mau a bwenzi langa mnyamatayo agogoda, nati, Nditsegulire, mlongwanga, wokondedwa wanga, nkhunda yanga, wangwiro wanga: Pakuti pamtu panga padzala mame, Patsitsi panga pali madontho a usiku.

3 Ndinayankha kuti, Ndabvula maraya anga, ndiwabvalenso bwanji? Ndatsuka mapazi anga; ndiwadetserenii?

4 Bwenzi langa analonga dzanja lace pazenera, Mtima wanga ndi kuguguda cifukwa ca iye,

5 Ndinauka ndikatsegulire bwenzi langa; Pamanja panga panakha nipa. Ndi pa zala zanga madzi a nipa, Pa zogwirira za mpikizo,

6 Ndinamtsegulira bwenzi langalo; Koma ndinampeza, bwenzi langa atacoka. Moyo wanga unalefuka polankhula iye: Ndinamfunafuna, osampeza; Ndinamuitana, koma sanandibvomera.

7 Alonda akuyenda m'mudzi anandipeza, Nandikantha, nanditema; Osunga maguta nandicotsera cophimba canga.

8 Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu, Mukapeza bwenzi langa, mudzamuuza ciani? Kuti ndadwala ndi cikondi.

9 Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji, Mkaziwe woposa kukongola? Bwenzi lako aposa abwenzi ena bwanji, Kuti utilumbirira motero?

10 Wokondedwa wanga ali woyera ndi wofiira, Womveka mwa zikwi khumi.

11 Mutu wace ukunga golidi, woyengetsa, Tsitsi lace lopotana, ndi lakuda ngati khungubwi.

12 Ana a maso ace akunga nkhunda pambali pa mitsinje ya madzi; Otsukidwa ndi mkaka, okhala pa mitsinje yodzala.

13 Masaya ace akunga citipula cabzyalamo ndiwo, Ngati mitumbira yoyangapo masamba onunkhira: Milomo yace ikunga akakombo, pakukhapo madzi a nipa.

14 Manja ace akunga zing'anda zagolidi zoikamo zonyezimira zoti biriwiri: Thupi lace likunga copanga ca minyanga colemberapo masafiro.

15 Miyendo yace ikunga zoimiritsa za mwala wonyezimira, Zogwirika m'kamwa mwa golidi: Maonekedwe ace akunga Lebano, okometsetsa ngati mikungudza.

16 M'kamwa mwace muli mokoma: inde, ndiye wokondweretsa ndithu. Ameneyu ndi wokondedwa wanga, ameneyu ndi bwenzi langa, Ana akazi inu a ku Yerusalemu.

6

1 Bwenzi lako wapita kuti, Mkaziwe woposa kukongola? Bwenzi lako wapambukira kuti, Tikamfunefune pamodzi nawe?

2 Bwenzi langa watsikira kumunda kwace, Ku zitipula za mphoka, Kukadya kumunda kwace, ndi kuchera akakombo.

3 Ndine wace wa wokondedwa wanga, wokondedwa wanganso ndiye wa ine; Aweta zace pakati pa akakombo.

4 Wakongola, bwenzi langa, namwaliwe ngati Tiriza, Wokoma ngati Yerusalemu, Woopsya ngati nkhondo ndi mbendera.

5 Undipambutsire maso ako, Pakuti andiopetsa. Tsitsi lako likunga gulu la mbuzi, Zigona pambali pa Gileadi.

6 Mano ako akunga gulu la nkhosa zazikazi, Zikwera kucokera kosamba; Yonse iri ndi ana awiri, Palibe imodzi yopoloza.

7 Palitsipa pako pakunga phande la khangaza Patseri pa cophimba cako.

8 Alipo akazi akulu a mfumu makumi asanu ndi limodzi, Kudza akazi ang'ono makumi asanu ndi atatu, Ndi anamwali osawerengeka.

9 Nkhunda yanga, wangwiro wangayu, ndiye mmodzi; Ndiye wobadwa yekha wa amace; Ndiye wosankhika wa wombala. Ana akazi anamuona, namucha wodala; Ngakhale akazi akulu a mfumu, ndi akazi ang'ono namtamanda.

10 Nati, Ndaniyo aturuka ngati mbanda kuca, Wokongola ngati mwezi, Woyera ngati dzuwa, Woopsya ngati nkhondo ndi mbendera?

11 Ndinatsikira ku munda wa ntedza, Kukapenya msipu wa m'cigwa, Kukapenya ngati pamipesa paphuka, Ngati pamakangaza patuwa maluwa.

12 Ndisanazindikire, moyo wanga unandiimika Pakati pa magareta a anthu anga aufulu.

13 Anati, Bwera, bwera, Msulamiwe; Bwera, bwera, tiyang'ane pa iwe. Muyang'aniranji pa Msulami, Ngati pa masewero akuguba?

7

1 Ha, mapazi ako akongola m'zikwakwata, Mwana wamkaziwe wa mfumu! Pozinga m'cuuno mwako pakunga zonyezimira, Nchito ya manja a mmisiri waluso.

2 Pamcombo pako pakunga cikho coulungika, Cosasowamo vinyo wosanganika: Pamimba pako pakunga mulu wa tirigu Wozingidwa ndi akakombo.

3 Maere ako akunga ana awiri a nswala Anabadwa limodzi.

4 Khosi lako likunga nsanja yaminyanga; Maso ako akunga matawale a ku Hesiboni, A pa cipata ca Batirabimu; Mphuno yako ikunga nsanja ya ku Lebano Imene iloza ku Damasiko.

5 Mutu wako ukunga Karimeli, Ndi tsitsi la pamtu pako likunga nsaru yakuda; Mfumu yamangidwa ndi nkhata zace ngati wamsinga.

6 Ha, ndiwe wokongola ndi wofunika, Bwenziwe, m'zokondweretsa!

7 Msinkhu wakowu ukunga mlaza, Maere ako akunga matsango amphesa,

8 Ndinati, Ndikakwera pamlazapo, Ndikagwira nthambi zace: Maere ako ange ngati matsango amphesa, Ndi kununkhira kwa mpweya wako ngati maula;

9 M'kamwa mwako munge ngati vinyo woposa, Womeza tseketeke bwenzi langa, Wolankhulitsa milomo ya ogona tulo.

10 Ndine wa wokondedwa wanga mnyamatayo, Ndine amene andifunayo.

11 Tiye, bwenzi langa, tinke kuminda; Titsotse m'miraga.

12 Tilawire kunka ku minda yamipesa; Tiyang'ane ngati mpesa waphuka, kunje ndi kuonetsa zipatso, Makangaza ndi kutuwa maluwa ace; Pompo ndidzakupatsa cikondi canga,

13 Mandimu anunkhira, Ndi pamakomo pathu zipatso zabwino, za mitundu mitundu, zakale ndi zatsopano, Zimene ndakukundikira iwe, wokondedwa wanga.

8

1 Mwenzi utakhala ngati mlongwanga, Woyamwa pa bere la amai! Ndikadakupeza panja, ndikadakupsompsona; Osandinyoza munthu.

2 Ndikadakutsogolera, kukulowetsa m'nyumba ya amai, Kuti andilange mwambo; Ndikadakumwetsa vinyo wokoleretsa, Ndi madzi a makangaza anga.

3 Dzanja lamanzere lace akadanditsamiritsa kumutu, Lamanja lace ndi kundifungatira.

4 Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu, Muutsiranji, mugalamutsiranji cikondi, Cisanafune mwini.

5 Ndaniyu acokera kucipululu, Alikutsamira bwenzi lace? Pa tsinde la muula ndinakugalamutsa mnyamatawe: Pomwepo amako anali mkusauka nawe, Pomwepo wakukubala anali m'pakati pa iwe.

6 Undilembe pamtima pako, mokhoma cizindikilo, nundikhomenso cizindikilo pamkono pako; Pakuti cikondi cilimba ngati imfa; Njiru imangouma ngati manda: Kung'anima kwace ndi kung'anima kwa moto, Ngati mphezi ya Yehova,

7 Madzi ambiri sangazimitse cikondi, Ngakhale mitsinje yodzala kucikokolola: Mwamuna akapereka katundu yense wa m'nyumba yace ngati sintho la cikondi, Akanyozedwa ndithu.

8 Tiri ndi mlongwathu wamng'ono, Alibe maere; Ticitirenji mlongwathu Tsiku lokhoma unkhoswe wace?

9 Ngati ndiye khoma, tidzamanga pa iye nsanja yasiliva: Ngati ndiye citseko tidzamtsekereza ndi matabwa amikungudza.

10 Ndine khoma, maere anga akunga nsanja zace: Pamaso pa mnyamatayo ndinafanana ngati wopeza mtendere.

11 Solomo anali ndi munda wamipesa ku Baalahamoni; Nabwereka alimi mundawo; Yense ambwezere ndalama cikwi cifukwa ca zipatso zace.

12 Koma munda wanga wamipesa, uli pamaso panga ndiwo wangatu; Naco cikwico, Solomo iwe, Koma olima zipatso zace azilandira mazana awiri.

13 Namwaliwe wokhala m'minda, Anzake amvera mau ako: Nanenso undimvetse.

14 Dzifulumira, mnyamatawe wokondedwa wanga, Dzifanane ngati mphoyo pena mwana wa mbawala Pa mapiri a mphoka,