1 IZI zinacitika masiku a Ahaswero, ndiye Ahasweroyo anacita ufumu kuyambira Indiya kufikira Kusi, pa maiko zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi awiri.
2 Masiku ajawo, pokhala Ahaswero pa mpando wa ufumu wace uli m'cinyumba ca ku Susani,
3 caka cacitatu ca ufumu wace, anakonzera madyerero akalonga ace onse, ndi omtumikira; amphamvu a Perisiya ndi Mediya, omveka ndi akalonga a maikowo anakhala pamaso pace,
4 pamene anaonetsa zolemera za ufumu wace waulemu, ndi ulemerero wa ukulu wace woposa, masiku ambiri, ndiwo masiku zana limodzi, mphambu makumi asanu ndi atatu.
5 Atatha masikuwa, mfumu inakonzera madyerero anthu onse okhala m'cinyumba ca ku Susani, akulu ndi ang'ono, masiku asanu ndi awiri, ku bwalo la munda wa maluwa wa ku cinyumba ca mfumu;
6 panali nsaru zolenjeka zoyera, zabiriwiri, ndi zamadzi, zomangika ndi zingwe za thonje labafuta, ndi lofiirira, pa zigwinjiri zasiliva, ndi nsanamira zansangalabwi; makama anali a golidi ndi siliva pa mayalidwe a miyala yofiira, ndi yoyera, ndi yoyezuka, ndi yakuda.
7 Nawapatsa cakumwa m'zomwera zagolidi, zomwerazo nzosiyana-siyana, ndi vinyo wacifumu anacuruka, monga mwa ufulu wa mfumu.
8 Ndi mamwedwewo anali monga mwa lamulo; panalibe kukakamiza; pakuti mfumu idaikira akulu onse a nyumba yace motero, kuti acite monga momwe akhumba ali yense.
9 Vasiti yemwe, mkazi wamkuru, anakonzera akazi madyerero m'nyumba yacifumu ya mfumu Ahaswero.
10 Tsiku lacisanu ndi ciwiri, pokondwera mtima wa mfumu ndi vinyo, iye anauza Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, ndi Abagita, Zetara, ndi Karikasi, adindo asanu ndi awiriwo akutumikira pamaso pa mfumu Ahaswero,
11 abwere naye Vasiti mkazi wamkuru pamaso pa mfumu ndi korona wacifumu, kuonetsa anthu ndi akuru kukoma kwace; popeza anali wokongola maonekedwe ace.
12 Koma Vasiti mkazi wamkuruyo anakana kudza pa mau a mfumu adamuuza adindowo; potero mfumu idapsa mtima ndithu, ndi mkwiyo wace unatentha m'kati mwace.
13 Pamenepo mfumu inanena kwa eni nzeru, akudziwa za m'tsogolo, mfumu idafotero nao onse akudziwa malamulo ndi maweruzo,
14 a pafupi naye ndiwo Karisena. Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena, ndi Memukana, akalonga asanu ndi awiri a Perisiya ndi Mediya, openya nkhope ya mfumu ndi kukhala oyamba m'ufumu.
15 Anati, Tidzacitanji naye mkazi wamkuru Vasiti monga mwa malamulo, popeza sanacita comuuza mfumu Ahaswero mwa adindo?
16 Ndi Memukana anati pamaso pa mfumu ndi akalonga, Vasiti mkazi wamkuru sanalakwira mfumu yekha, komanso akalonga onse, ndi mitundu yonse ya anthu okhala m'maiko onse a mfumu Ahaswero.
17 Pakuti macitidwe awa a mkazi wamkuruyo adzabuka kufikira akazi onse, kupeputsa amuna ao pamaso pao; anthu akati, Mfumu Ahaswero anati abwere naye Vasiti mkazi wamkuru pamaso pace, koma sanadza iye.
18 Inde tsiku lomwelo akazi akuru a Perisiya ndi Mediya, atamva macitidwe a mkazi wamkuruyo, adzatero nao momwemo kwa akalonga onse a mfumu. Ndi cipeputso ndi mkwiyo zidzacuruka.
19 Cikakomera mfumu, aturuke mau acifumu pakamwa pace, nalembedwe m'malamulo a Aperisiya ndi Amediya, angasinthike, kuti Vasiti asalowenso pamaso pa mfumu Ahaswero; ndi mfumu aninkhe cifumu cace kwa mnzace womposa iye.
20 Ndipo mau amene adzaika mfumu akamveka m'ufumu wace wonse, (pakuti ndiwo waukuru), akazi onse adzacitira amuna ao ulemu, akulu ndi ang'ono.
21 Ndipo mauwo anakonda mfumu ndi akalonga; ndi mfumu inacita monga mwa mau a Memukana,
22 natumiza akalata ku maiko onse a mfumu, ku dziko liri lonse monga mwa cilembedwe cao, ndi ku mtundu uli wonse monga mwa cinenedwe cao, kuti mwamuna ali yense akhale wamkuru m'nyumba yace yace, nawabukitse monga mwa cinenedwe ca anthu amtundu wace.
1 Zitatha izi, utaleka mkwiyo wa mfumu Ahaswero, anakumbukila Vasiti, ndi cocita iye, ndi comlamulidwira.
2 Pamenepo anyamata a mfumu omtumikira anati, Amfunire mfumu anamwali okongola;
3 ndi mfumu aike oyang'anira m'maiko onse a ufumu wace, kuti asonkhanitse anamwali onse okongola m'cinyumba ca ku Susani, m'nyumba ya akazi; awasunge Hege mdindo wa mfumu wosungira akazi, nawapatse zowayeretsa;
4 ndi namwali womkonda mfumu akhale mkazi wamkuru m'malo mwa Vasiti. Ndipo cinthuci cinamkonda mfumu, nacita comweco.
5 Panali Myuda m'cinyumba ca ku Susani, dzina lace ndiye Moredekai, mwana wa Yairi, mwana wa Simei, mwana wa Kisi Mbenjamini;
6 uyu anatengedwa ndende ku Yerusalemu, pamodzi ndi andende anatengedwa pamodzi ndi Yekoniya mfumu ya Yuda, amene Nebukadinezara mfumu ya Babulo adamtenga ndende.
7 Ndipo iye adalera Hadasa, ndiye Estere, mwana wamkazi wa atate wace wamng'ono; popeza iye analibe atate kapena amai; ndi namwaliyo anali wa maonekedwe okoma, ndi wokongola; ndipo atamwalira atate wace ndi mai wace, Moredekai anamtenga akhale mwana wace.
8 Ndipo kunali, atamveka mau a mfumu ndi lamulo lace, ndipo atasonkhanidwa anamwali ambiri m'cinyumba ca ku Susani, awasunge Hege, anamtenga Estere yemwe, alowe m'nyumba ya mfumu, amsunge Hege wosunga akazi.
9 Ndipo namwaliyo anamkomera, namcitira cifundo; ndipo anafulumira kumpatsa zace zomyeretsa, ndi magawo ace, ndi anamwali asanu ndi awiri oyenera kumpatsa ocokera m'nyumba ya mfumu; ndipo anamsuntha iye ndi anamwali ace akhale m'malo okometsetsa m'nyumba ya akazi.
10 Estere sadaulula mtundu wace ndi cibale cace; pakuti Moredekai adamuuzitsa kuti asadziulule.
11 Ndi Moredekai akayendayenda tsiku ndi tsiku ku bwalo la nyumba ya akazi, kuti adziwe umo akhalira Estere, ndi cimene cidzamcitikira.
12 Kunafika tsono kulowa kwace kwa namwali ali yense, kuti alowe kwa mfumu Ahaswero, atamcitira monga mwa lamulo la akazi, miyezi khumi ndi iwiri; pakuti adafokwaniritsa masiku a mayeretsedwe ao motero, miyezi isanu ndi umodzi ndi mafuta a mure, ndi miyezi isanu ndi umodzi ndi zonunkhira bwino, ndi zoyeretsa akazi.
13 Ndipo namwali ali yense analowa kwa mfumu matero, ziri zonse anafuna anampatsa zocokera m'nyumba ya akazi, alowe nazo ku nyumba ya mfumu.
14 Madzulo ace analowamo, nabwera m'mawa mwace kumka ku nyumba yaciwiri ya akazi, amsunge Saasigazi mdindo wa mfumu, wosunga akazi ang'ono a mfumu; iyeyu sanakwanso kwa mfumu, koma akakondwera naye mfumu, ndi kumuitana kumchula dzina lace, ndiko.
15 Pofika tsono kulowa kwace kwa Estere mwana wa Abihaili, atate wamng'ono wa Moredekai, amene adadzitengera akhale mwana wace, kuti alowe kwa mfumu, sanafuna kanthu koma zonena Hege mdindo wa mfumu wosunga akazi ndizo. Ndipo Estere anayamikizidwa pamaso pa onse ompenya.
16 Momwemo anatengedwa Estere kumka kwa mfumu Ahaswero, ku nyumba yace yacifumu, mwezi wakhumi, ndiwo mwezi wa Tebete, caka cacisanu ndi ciwiri ca ufumu wace.
17 Ndipo mfumu inakonda Estere koposa akazi onse, nalandira iye kuyanja ndi cifundo pamaso pace, koposa anamwali onse; motero anaika korona wacifumu pamutu pace, namuyesa mkazi wamkuru m'malo mwa Vasiti.
18 Pamenepo mfumu inawakonzera madyerero akuru ace onse, ndi omtumikira, ndiwo madyerero a Estere; napumulitsa maiko, naninkha zaufulu monga mwa ufulu wa mfumu.
19 Ndipo posonkhanidwa anamwali nthawi yaciwiri Moredekai anali wa m'bwalo la mfumu.
20 Estere sadaulula cibale cace kapena mtundu wace, monga Moredekai adamuuza; popeza Estere anacita mau a Moredekai monga m'mene analeredwa naye.
21 Masiku awa pokhala Moredekai wa m'bwalo la mfumu, Bigitana ndi Teresi, adindo awiri a mfumu osunga pakhomo, anapsa mtima, nayesa kumthira manja mfumu Ahaswero.
22 Koma cidadziwika ici kwa Moredekai, ndiye anafotokozera Estere mkazi wamkuru; ndi Estere anamuuza mfumu, kumnenera Moredekai.
23 Ndipo atafunsira mlanduwo, anaupeza momwemo, napacikidwa onse awiri pamtengo; ndipo anacilemba m'buku la mbiri pamaso pa mfumu.
1 Zitatha izi, mfumu Ahaswero anamkuza Hamani mwana wa Hamedata, wa ku Agagi, namkweza, naika mpando wace upose akalonga onse okhala naye.
2 Ndipo anyamata onse a mfumu okhala m'cipata ca mfumu anamweramira, namgwadira Hamani; pakuti mfumu idalamulira cotero za iye. Koma Moredekai sanamweramira kapena kumgwadira.
3 Ndipo anyamata a mfumu okhala m'cipata ca mfumu anati kwa Moredekai, Ulakwiranji pa lamulo la mfumu?
4 Kunali tsono, pomalankhula naye tsiku ndi tsiku, osawamvera iye, anauza Hamani, kuona ngati mlandu wa Moredekai udzakoma; popeza iye adawauza kuti ali Myuda.
5 Ndipo Hamani, pakuona kuti Moredekai sanamweramira kapena kumgwadira, mtima wace unadzala mkwiyo.
6 Koma anaciyesa copepuka kumthira manja Moredekai yekha; pakuti adamfotokozera mtundu wace wa Moredekai; potero Hamani anafuna kuononga Ayuda lonse okhala m'ufumu wonse wa Ahaswero, ndiwo a mtundu wa Moredekai.
7 Mwezi woyamba ndiwo mwezi wa Nisani, caka cakhumi ndi ciwiri ca mfumu Ahaswero, anaombeza Puri, ndiwo ula, pamaso pa Hamani tsiku ndi tsiku, mwezi ndi mwezi, mpaka mwezi wakhumi ndi ciwiri, ndiwo mwezi wa Adara.
8 Ndipo Hamani anati kwa mfumu Ahaswero, Pali mtundu wina wa anthu obalalika ndi ogawanikana mwa mitundu ya anthu m'maiko onse a ufumu wanu, ndi malamulo ao asiyana nao a anthu onse, ndipo sasunga malamulo a mfumu; cifukwa cace mfumu siiyenera kuwaleka.
9 Cikakomera mfumu, cilembedwe kuti aonongeke iwo; ndipo ndidzapereka matalente a siliva zikwi khumi m'manja a iwo akusunga nchito ya mfumu, abwere nao kuwaika m'nyumba za cuma ca mfumu.
10 Ndipo mfumu inabvula mphete yace pa cala cace, naipereka kwa Hamani mwana wa Hamedata wa ku Agagi, mdani wa Ayuda.
11 Ndipo mfumu idati kwa Hamani, Siliva akhale wako, ndi anthu omwe; ucite nao monga momwe cikukomera.
12 Pamenepo anaitana alembi a mfumu mwezi woyamba, tsiku lace lakhumi ndi citatu, nalembera monga mwa zonse Hamani analamulira akazembe ndi ziwanga zoyang'anira maiko ali onse, ndi akalonga a mitundu iri yonse ya anthu, maiko ali onse monga mwa cilembedwe cao, ndi mitundu iri yonse ya anthu monga mwa cinenedwe cao; anazilemba m'dzina la mfumu Ahaswero, nazisindikiza ndi mphete ya mfumu.
13 Ndipo anatumiza akalata ndi amtokoma ku maiko onse a mfumu, kuti aononge, aphe, napulule Ayuda onse, ndiwo ana, ndi okalamba, makanda, ndi akazi, tsiku limodzi, ndilo tsiku lakhumi ndi citatu la mwezi wakhumi ndi ciwiri, ndiwo mwezi wa Adara; nalande zao mofunkha.
14 Mau a colembedwaco, ndiwo kuti licitike lamulo m'maiko onse, analalikidwa kwa anthu onse, kuti akonzekeretu tsiku lomwelo.
15 Amtokoma anaturuka ofulumizidwa ndi mau a mfumu, ndi lamulo linabukitsidwa m'cinyumba ca ku Susani; ndipo mfumu ndi Hamani anakhala pansi kumwa; koma mudzi wa Susani unadodoma.
1 Koma podziwa Moredekai zonse zidacitikazi, Moredekai anang'amba zobvala zace, nabvala ciguduli ndi mapulusa, naturuka pakati pa mudzi, napfuula, nalira kulira kwakukuru ndi kowawa,
2 nafika popenyana ndi cipata ca mfumu; popeza sanathe munthu kulowa ku cipata ca mfumu wobvala ciguduli.
3 Ndi m'maiko monse, pali ponse anafikapo mau a mfumu ndi lamulo lace, panali maliro akuru mwa Ayuda, ndi kusala, ndi kulira misozi, ndi kubuma; nagona m'ciguduli ndi mapulusa ambiri.
4 Ndipo anamwali a Estere ndi adindo ace anadza, namuuza; ndi mkazi wamkuru anawawidwa mtima kwambiri, natumiza cobvala abveke Moredekai, ndi kumcotsera ciguduli cace; koma sanacilandira.
5 Pamenepo Estere anaitana Hataki mdindo wina wa mfumu, amene idamuika amtumikire, namuuza amuke kwa Moredekai, kuti adziwe ici nciani ndi cifukwa cace ninji.
6 Naturuka Hataki kumka kwa Moredekai ku khwalala la mudzi linali popenyana ndi cipata ca mfumu.
7 Ndipo Moredekai anamfotokozera zonse zidamgwera, ndi mtengo wace wa ndarama adati Hamani adzapereka m'nyumba ya cuma ca mfumu pa Ayuda, kuwaononga.
8 Anampatsanso citsanzo ca lamulo lolembedwa adalibukitsa m'Susani, kuwaononga, acionetse kwa Estere, ndi kumfotokozera, ndi kumlangiza alowe kwa mfumu, kumpembedza, ndi kupempherera anthu ace kwa iye.
9 Nadza Hataki, namuuza Estere mau a Moredekai.
10 Pamenepo Estere ananena ndi Hataki, namtuma akauze Moredekai, ndi kuti,
11 Akapolo onse a mfumu ndi anthu a m'maiko a mfumu adziwa kuti ali yense, ngakhale wamwamuna kapena wamkazi, akalowa kwa mfumu ku bwalo la m'katimo wosaitanidwa, lamulo la pa iye ndi limodzi, ndilo kuti amuphe, akapanda mfumu kumloza ndi ndodo yacifumu yagolidi kuti akhale ndi moyo; koma ine sanaodiitana ndilowe kwa mfumu masiku awa makumi atatu.
12 Ndipo anamuuza Moredekai mau a Estere.
13 Koma Moredekai anawauza ambwezere mau Estere, kuti, Usamayesa m'mtima mwako kuti udzapulumuka m'nyumba ya mfumu koposa Ayuda onse ena.
14 Pakuti ukakhala cete konse tsopano lino, cithandizo ndi cipulumutso zidzafuma kwina; koma iwe ndi nyumba ya atate wako mudzaonongeka; ndipo kaya, kapena walowera ufumu cifukwa ca nyengo yonga iyi.
15 Pamenepo Estere anati ambwezere mau Moredekai,
16 Muka, sonkhanitsa Ayuda onse opezeka m'Susani, nimundisalire, osadya osamwa masiku atatu, usiku ndi usana, ine ndemwe ndi anamwali anga tidzasala momwemo, ndipo motero ndidzalowa kwa mfumu, ndiko kosalingana ndi lamulo; ndikaonongeka tsono ndionongeke,
17 Napita Moredekai, nacita monga mwa zonse adamlamulira Estere.
1 Ndipo kunali tsiku lacitatu, Estere anabvala zobvala zace zacifumu, nakaimirira m'bwalo la m'kati la nyumba ya mfumu, popenyana pa nyumba ya mfumu; ndi mfumu inakhala pa mpando wace wacifumu m'nyumba yacifumu, pandunji polowera m'nyumba.
2 Ndipo kunali, pamene mfumu inaona Estere mkazi wamkuruyo alikuima m'bwalo, inamkomera mtima; ndi mfumu inamloza Estere ndi ndodo yacifumu yagolidi inali m'dzanja lace. Nayandikira Estere, nakhudza nsonga ya ndodoyo.
3 Ninena naye mfumu, Mufunanji, Estere mkazi wamkuru? pempho lanu nciani? lidzaperekedwa kwa inu, kufikira limodzi la magawo awiri a ufumuwo.
4 Ndipo Estere anati, Cikakomera mfumu, adze mfumu ndi Hamani lero ku madyerero ndinawakonzera.
5 Niti mfumu, Mumfulumize Hamani, acitike mau a Estere. Nidza mfumu ndi Hamani ku madyerero adawakonzera Estere.
6 Ndipo mfumu inati kwa Estere pa madyerero a vinyo, Pempho lanu nciani? lidzaperekedwa kwa inu; mufunanji? cidzacitika, kufikira limodzi la magawo awiri a ufumuwo.
7 Nayankha Estere, nati, Pempho langa ndi kufuna kwanga ndiko,
8 ngati mfumu indikomera mtima, ngatinso cakomera mfumu kupereka pempho langa ndi kucita cofuna ine, adze mfumu ndi Hamani ku madyerero ndidzawakonzera; ndipo mawa ndidzacita monga yanena mfumu.
9 Ndipo Hamani anaturuka tsiku lomwelo wosekerera ndi wokondwera mtima; koma pamene Hamani anapenya Moredekai ku cipata ca mfumu, osamnyamukira kapena kumfumukira, Hamani anadzazidwa ndi mkwiyo pa Moredekai.
10 Koma Hamani anadziletsa, namuka kwao, natumiza munthu kukatenga mabwenzi ace, ndi Zeresi mkazi wace.
11 Nawawerengera Hamani kulemera kwace kwakukuru, ndi ana ace ocuruka, ndi zonse mfumu idamkuza nazo, ndi umo adamkweza koposa akalonga ndi anyamata a mfumu.
12 Hamani anatinso, Ndiponso Estere mkazi wamkuru sanalola mmodzi yense alowe pamodzi ndi mfumu ku madyerero adakonzawo, koma ine ndekha; nandiitana mawanso pamodzi ndi mfumu.
13 Koma zonsezi sindipindula nazo kanthu konse, pokhala ndirikuona Moredekai Myudayo alikukhala ku cipata ca mfumu.
14 Pamenepo Zeresi mkazi wace, ndi mabwenzi ace onse ananena naye, Apange mtengo, msinkhu wace mikono makumi asanu, ndi mawa mukanene nayo mfumu kuti ampacike Moredekai pamenepo; nimulowe pamodzi ndi mfumu kumadyerero wokondwera. Ndipo ici cidakomera Hamani, napangitsa anthu mtengowo.
1 Usiku uja tulo tidamwazikira mfumu, niti abwere nalo buku la mbiri, naliwerenga pamaso pa mfumu.
2 Napeza mudalembedwa kuti Moredekai adaulula za Bigitana ndi Teresi, awiri a adindo a mfumu osunga pakhomo, amene adayesa kumthira manja mfumu Ahaswero.
3 Niti mfumu, Anamcitira Moredekai ulemu ndi ukulu wotani cifukwa ca ici? Ndipo anyamata a mfumu akuitumikira ananena nayo, Sanamcitira kanthu.
4 Niti mfumu, Ali kubwalo ndani? Koma Hamani adalowa m'bwalo lakunja la nyumba ya mfumu kulankhula ndi mfumu za kupacika Moredekai pamtengo adaukonzeratu.
5 Ndipo anyamata a mfumu ananena nayo, Taonani, Hamani alikuima pabwalo. Niti mfumu, Alowe.
6 Nalowa Hamani. Ndipo mfumu inati kwa iye, Kodi amcitire ciani munthu amene mfumu ikondwera kumcitira ulemu? Ndipo Hamani anati mumtima mwace, Ndaniyo mfumu ikondwera kumcitira ulemu koposa ine?
7 Nati Hamani kwa mfumu, Munthu amene mfumu ikondwera kumcitira ulemu,
8 amtengere cobvala cacifumu amacibvala mfumu, ndi kavalo amakwerapo mfumu, naike korona wacifumu pamutu pace,
9 napereke cobvala ndi kavalo m'dzanja la wina womveketsa wa akalonga a mfumu, nabveke naco munthu amene mfumu ikondwera kumcitira ulemu, namuyendetse pa kavaloyo m'khwalala la m'mudzi, napfuule pamaso pace, Azitero naye munthu amene mfumu ikondwera kumcitira ulemu.
10 Pamenepo mfumu inati kwa Hamani, Fulumira, tenga cobvala ndi kavalo monga umo wanenera, nucitire cotero Moredakai Myudayo, wokhala pa cipata ca mfumu; kasasowepo kanthu ka zonse wazinena.
11 Ndipo Hamani anatenga cobvala ndi kavalo, nabveka Moredekai, namuyendetsa pa kavalo m'khwalala la m'mudzi, napfuula pamaso pace, Azitero naye munthu amene mfumu ikondwera kumcitira ulemu.
12 Ndipo Moredekai anabweranso ku cipata ca mfumu. Koma Hamani anafulumira kumka kwao, wacisoni ndi wopfunda mutu wace.
13 Ndipo Hamani anafotokozera Zeresi mkazi wace, ndi mabwenzi ace onse, zonse zidamgwera, Nanena naye anzeru ace, ndi Zeresi mkazi wace, Moredekai amene wayamba kutsika pamaso pace, akakhala wa mbumba ya Ayuda, sudzamlaka; koma udzagwada pamaso pace.
14 Akali cilankhulire naye, anafika adindo a mfumu, nafulumira kumtenga Hamani kumka naye kumadyerero adawakonzera Estere.
1 Motero inadza mfumu ndi Hamani kumwa naye mkazi wamkuru Estere.
2 Nitinso mfumu kwa Estere tsiku laciwirili pa madyerero a vinyo, Pempho lanu nciani, mkazi wamkuru Estere? lidzapatsidwa kwa inu; mufunanji? cidzacitika, kufikira limodzi la magawo awiri a ufumu wanga.
3 Nayankha mkazi wamkuru Estere, nati, Ngati mwandikomera mtima, mfumu, ndipo cikakomera mfumu, andilekere moyo wanga pa kupempha kwanga, ndi wa anthu a mtundu wanga pa pempho langa;
4 pakuti tagulitsidwa; ine ndi anthu amtundu wanga, kuti ationonge, atiphe, natipulule, Koma tikadagulitsidwa tikhale akapolo ndi adzakazi, ndikadakhala cete; cinkana wosautsa sakadakhoza kubwezera kusowa kwa mfumu.
5 Pamenepo mfumu Ahaswero inalankhula, niti kwa mkazi wamkuru Estere, Ndani uyu, ali kuti iyeyu wadzazidwa mtima wace kuti azitero?
6 Nati Estere, Munthu wosautsa ndi mdani ndiye Hamani woipa uyu. Pamenepo Hamani anagwidwa mantha pamaso pa mfumu ndi mkazi wamkuru.
7 Ninyamuka mfumu mu mkwiyo wace ku madyerero a vinyo, nimka ku munda wa maluwa wa kucinyumba; koma Hamani anatsalira kudzipempherera moyo kwa mkazi wamkuru Estere; popeza anapenya kuti mfumu inatsimikiza mtima kumcitira coipa.
8 Nibwera mfumu ku munda wa maluwa wa kucinyumba kulowanso m'nyumba munali madyerero a vinyo, napeza Hamani atagwa pa kama wokhalapo Estere. Niti mfumu, Kodi aumiriza mkazi wamkuru pamaso panga m'nyumba? Poturuka mau pakamwa pa mfumu anamphimba Hamani nkhope.
9 Nati Haribona wina wa adindo okhala pamaso pa mfumu, Taonaninso, mtengowo msinkhu wace mikono makumi asanu, umene Hamani anaupangira Moredekai wonenera mfumu zokoma, uimiritsidwa m'nyumba ya Hamani. Niti mfumu, Mpacike pomwepo.
10 Nampacika Hamani pa mtengo adaukonzera Moredekai. Pamenepo mkwiyo wa mfumu unatsika.
1 Tsiku lomwelo mfumu Ahaswero anampatsa mkazi wamkuru Estere nyumba ya Hamani mdani wa Ayuda, Nafika Moredekai pamaso pa mfumu; pakuti Estere adamuuza za cibale cace.
2 Ndipo mfumu inabvula mphete yace adailanda kwa Hamani, naipereka kwa Moredekai. Ndi Estere anaika Moredekai akhale woyang'anira nyumba ya Hamani.
3 Nanenanso Estere pamaso pa mfumu, nagwa ku mapazi ace, nalira misozi, nampembedza kuti acotse coipaco ca Hamani wa ku Agagi, ndi ciwembu adacipangira Ayuda,
4 Ndipo mfumu inaloza Estere ndi ndodo yacifumu yagolidi. Nanyamuka Estere, naima pamaso pa mfumu.
5 Nati, Cikakomera mfumu, ndipo ngati yandikomera mtima, niciyenera kwa mfumu, ngatinso ndimcititsa kaso, alembere cosintha mau a akalata a ciwembu ca Hamani mwana wa Hamedata wa ku Agagi, amene adawalembera kuononga Ayuda okhala m'maiko onse a mfumu;
6 pakuti ndidzapirira bwanji pakuciona coipa cirikudzera amtundu wanga, kapena ndidzapirira bwanji pakuciona cionongeko ca pfuko langa?
7 Pamenepo mfumu Ahaswero anati kwa mkazi wamkuru Estere, ndi kwa Moredekai Myuda, Taonani, ndampatsa Estere nyumba ya Hamani, ndi iyeyu anampacika pamtanda, cifukwa anaturutsa dzanja lace pa Avuda,
8 Mulembere inunso kwa Ayuda monga mufuna, m'dzina la mfumu, nimusindikize ndi mphete ya mfumu; pakuti kalata wolembedwa m'dzina la mfumu, ndi kusindikizika ndi mphete ya mfumu, palibe munthu akhoza kumsintha.
9 Pamenepo anaitana alembi a mfumu nthawi yomweyo, mwezi wacitatu, ndiwo mwezi wa Sivani, tsiku lace la makumi awiri ndi citatu, monga mwa zonse Moredekai analamulira; nalembera kwa Ayuda ndi kwa akazembe, ndi ziwanga, ndi akalonga a kumaiko, oyambira ku Indiya, ofikira ku Kusi, maiko zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi awiri, ku dziko liri lonse monga mwa cilembedwe cao, ndi mtundu uli wonse monga mwa cinenedwe cao, ndi kwa Ayuda monga mwa cilembedwe cao, ndi monga mwa cinenedwe cao.
10 Ndipo analembera m'dzina la mfumu Ahaswero, nasindikiza ndi mphete ya mfumu, natumiza akalata ndi amtokoma pa akavalo, okwera pa akavalo aliwiro acifumu, obadwa mosankhika;
11 m'menemo mfumu inalola Ayuda okhala m'midzi iri yonse asonkhane, ndi kulimbikira moyo wao, kuononga, kupha, ndi kupulula mphamvu yonse ya anthu ndi ya dziko yofuna kuwathira nkhondo, iwo, ana ang'ono ao, ndi akazi ao, ndi kulanda zofunkha zao,
12 tsiku lomwelo, m'maiko onse a mfumu Ahaswero, tsiku lakhumi ndi citatu la mwezi wakhumi ndi ciwiri, ndiwo mwezi wa Adara.
13 Citsanzo cace, ca lemboli, cakuti abukitse lamulo m'maiko onse, cinalalikidwa kwa mitundu yonse ya anthu, kuti, Ayuda akonzekeretu tsiku lijalo, kubwezera cilango adani ao.
14 Naturuka amtokoma okwera pa akavalo aliwiro acifumu; pakuti mau a mfumu anawafulumiza ndi kuwaumiriza; ndipo lamulolo linabukitsidwa m'cinyumba ca ku Susani.
15 Ndipo Moredekai anaturuka pamaso pa mfumu wobvala cobvala cacifumu camadzi ndi coyera, ndi korona wamkuru wagolidi, ndi maraya abafuta ndi ofiirira; ndi mudzi wa Susani unapfuula ndi kukondwera.
16 Ayuda anali nako kuunika, ndi kukondwera, ndi cimwemwe, ndi ulemu.
17 Ndi m'maiko monse, ndi m'midzi yonse, mudafika mau a mfumu ndi lamulo lace, Ayuda anali nako kukondwera ndi cimwemwe, madyerero ndi tsiku lokoma. Ndipo ambiri a mitundu ya anthu a m'dziko anasanduka Ayuda; pakuti kuopsa kwa Ayuda kudawagwera.
1 Mwezi wakhumi ndi ciwiri tsono, ndiwo mwezi wa Adara, tsiku lace lakhumi ndi citatu, mau a mfumu ndi lamulo lace ali pafupi kucitika, tsikuli adani a Ayuda anayesa kuwacitira ufumu, koma cinasinthika; popeza Ayuda anacitira ufumu iwo odana nao;
2 pakuti Ayuda anasonkhana pamodzi m'midzi mwao, m'maiko onse a mfumu Ahaswero, kuwathira manja ofuna kuwacitira coipa, ndipo palibe munthu analimbika pamaso pao; popeza kuopsa kwao kudawagwera mitundu yonse ya anthu.
3 Ndipo akalonga onse a maikowo, ndi akazembe, ndi ziwanga, ndi iwo ocita nchito ya mfumu, anathandiza Ayuda; popeza kuopsa kwa Moredekai kudawagwera.
4 Pakuti Moredekai anali wamkuru m'nyumba ya mfumu, ndi mbiri yace idabuka m'maiko onse; pa kuti munthuyu Moredekai anakula-kulabe.
5 Ndipo Ayuda anakantha adani ao onse, kuwakantha ndi lupanga, ndi kuwapulula, nacitira odana nao monga anafuna.
6 Ndipo m'cinyumba ca ku Susani Ayuda anakantha, naononga amuna mazana asanu.
7 Napha Parisandata, ndi Dalifoni, ndi Asipata,
8 ndi Porata, ndi Adaliya, ndi Aridata,
9 ndi Parimasta, ndi Arisai, ndi Aridai, ndi Vaisata,
10 ana amuna khumi a Hamani mwana wa Hamedata, mdani wa Ayuda. Koma sanalanda zofunkha.
11 Tsiku lomwelo anabwera naco kwa mfumu ciwerengo ca iwo ophedwa m'cinyumba ca ku Susani.
12 Ndipo mfumu inati kwa mkazi wamkuru Estere, Ayuda adapha, naononga amuna mazana asanu m'cinyumba ca ku Susani, ndi ana amuna khumi a Hamani; nanga m'maiko ena a mfumu munacitikanji? pempho lanu ndi ciani tsono? lidzacitikira inu; kapena mufunanjinso? kudzacitika.
13 Nati Estere, Cikakomera mfumu, alole Ayuda okhala m'Susani acite ndi mawa lomwe monga mwa lamulo la lero; ndi ana amuna khumi a Hamani apacikidwe pamtengo.
14 Ndipo mfumu inati azicita motero, nalamulira m'Susani, napacikidwa ana amuna khumi a Hamani.
15 Ndipo Ayuda okhala m'Susani anasonkhana pamodzi, tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi wa Adara, napha amuna mazana atatu m'Susani; koma sanalanda zofunkha.
16 Nasonkhana pamodzi Ayuda ena okhala m'maiko a mfumu, nalimbikira moyo wao, napumula pa adani ao, nawapha a iwo odana nao zikwi makumi asanu ndi awiri mphambu zisanu; koma sanalanda zofunkha.
17 Cinacitika ici tsiku lakhumi ndi citatu la mwezi wa Adara, ndi tsiku lace lakhumi ndi cinai anapumula, naliyesa tsiku lamadyerero ndi lakukondwesa.
18 Koma Ayuda okhala m'Susani anasonkhana tsiku lace lakhumi ndi citatu ndi lakhumi ndi cinai, ndi pa tsiku lakhumi ndi cisanu anapumula, naliyesa tsiku lamadyerero ndi lakukondwera.
19 Cifukwa cace Ayuda a kumiraga, okhala m'midzi yopanda malinga, amaliyesa tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi wa Adara tsiku la kukondwera ndi madyerero, ndi tsiku lokoma, ndi lakutumizirana magawo.
20 Ndipo Moredekai analembera izi, natumiza akalata kwa Ayuda onse okhala m'maiko onse a mfumu Ahaswero, a kufupi ndi a kutali,
21 kuwalimbikitsira, asunge tsiku lakhumi ndi cinai, mwezi wa Adara, ndi tsiku lace lakhumi ndi cisanu lomwe, caka ndi caka,
22 ndiwo masiku amene Ayuda anapumula pa adani ao; ndi mwezi wacisoni unawasandulikira wakukondwera, ndi wamaliro ukhale tsiku lokoma, awayese masiku amadyerero ndi akukondwera, akutumizirana magawo, ndi akupatsa zaufulu kwa osauka.
23 Ndipo Ayuda anabvomereza kucita monga umo adayambira, ndi umo Moredekai adawalembera;
24 popeza Hamani mwana wa Hamedata wa ku Agagi, mdani wa Ayuda onse, adapangira Ayuda ciwembu kuwaononga, naombeza Puri, ndiwo ula, kuwatha ndi kuwaononga;
25 koma pofika mlanduwo kwa mfumu, anati mwa akalata kuti ciwembu cace coipa adacipangira Ayuda, cimbwerere mwini; ndi kuti Iye ndi ana amuna ace apacikidwe pamtengo,
26 Cifukwa cace anacha masikuwa Purimu, ndilo dzina la ulawo. Momwemo, cifukwa ca mau onse a kalatayo, ndi izi adaziona za mlanduwo, ndi ici cidawadzera,
27 Ayuda anakhazikitsa ici, nadzilonjezetsa okha, ndi mbeu yao, ndi onse akuphatikana nao, cingalekeke, kuti adzasunga masiku awa awiri monga mwalembedwa, ndi monga mwa nyengo yao yoikika, caka ndi caka;
28 ndi kuti masikuwa adzakumbukika ndi kusungika mwa mibadwo yonse, banja liri lonse, dziko liri lonse, ndi mudzi uli wonse; ndi kuti masiku awa sadzalekeka mwa Ayuda, kapena kusiyidwa cikumbukilo cao mwa mbeu yao.
29 Pamenepo Estere mkazi wamkuru mwana wa Abihaili, ndi Moredekai Myuda, analembera molamulira, kukhazikitsa kalata uyu waciwiri wa Purimu.
30 Natumiza iye akalata kwa Ayuda onse, ku maiko zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi awiri a ufumu wa Ahaswero, ndiwo mau a mtendere ndi coonadi;
31 kukhazikitsa masiku awa a Purimu m'nyengo zao, m'mene Moredekai Myuda ndi mkazi wamkuru Estere adawakhazikitsira; ndi umo anadzikhazikitsira okha, ndi mbeu yao, kunena za kusala kwao, ndi kupfuula kwao.
32 Ndipo kunena kwace kwa Estere kunakhazikitsa mau awa a Purimu; ndipo kunalembedwa m'buku.
1 Ndipo mfumu Ahaswero inasonkhetsa dziko, ndi zisumbu za ku nyanja yamcere.
2 Ndi zocita zonse za mphamvu yace, ndi nyonga zace, ndi mafotokozedwe a ukulu wa Moredekai, umene mfumu inamkulitsa nao, sizilembedwa kodi m'buku la mbiri ya mafumu a Mediya ndi Perisiya?
3 Pakuti Moredekai Myuda anatsatana naye mfumu Ahaswero, nakhala wamkuru mwa Ayuda, nabvomerezeka mwa unyinji wa abale ace wakufunira a mtundu wace zokoma, ndi wakunena za mtendere kwa mbeu yace yonse.