1 PAULO, mtumwi wa Kristu Yesu monga mwa cilamuliro ca Mulungu Mpulumutsi wathu, ndi ca Kristu Yesu, ciyembekezo cathu:
2 kwa Timoteo mwana wanga weniweni m'cikhulupiriro: Cisomo, cifundo, mtendere za kwa Mulungu Atate ndi kwa Kristu Yesu Ambuye wathu.
3 Monga ndinakudandaulira iwe utsalire m'Efeso, popita ine ku Makedoniya, nditeronso, kuti ukalamulire ena ajawa asaphunzitse kanthu kena,
4 kapena asasamale nkhani zacabe, ndi mawerengedwe osalekeza a mafuko a makolo, ndiwo akuutsa mafunso, osati za udindo wa Mulungu umene uli m'cikhulupiriro;
5 koma citsirizo ca cilamuliro ndico cikondi cocokera mu mtima woyera ndi m'cikumbu mtima cokoma ndi cikhulupiriro cosanyenga;
6 zimenezo, ena pozilambalala anapatukira kutsata mau opanda pace;
7 pofuna kukhala aphunzitsi a lamulo ngakhale sadziwitsa zimene azmena, kapena azilimbikirazi.
8 Koma mudziwa kuti lamulo ndi labwino, ngati munthu acita nalo monga mwa lamulo,
9 podziwa ici, kuti lamulo siliikika kwa munthu wolungama, koma kwa osayeruzika ndi osamvera lamulo, osapembedza, ndi ocimwa, osalemekeza ndi amnyozo, akupha atate ndi akupha amai, akupha anzao,
10 acigololo, akucita zoipa ndi amuna, akuba anthu, amabodza, olumbira zonama, ndipo ngati kuli kena kakutsutsana naco ciphunzitso colamitsa;
11 monga mwa Uthenga Wabwino wa ulemerero wa Mulungu wolemekezeka, umene anandisungitsa ine.
12 Ndimyamika iye wondipatsa ine mphamvu, ndiye Kristu Yesu, Ambuye wathu, kuti anandiyesa wokhulupirika, nandiika kuutumiki,
13 ndingakhale kale ndinali wamwano, ndi wolondalonda, ndi wacipongwe; komatu anandicitira cifundo, popeza ndinazicita wosazindikira, wosakhulupirira;
14 koma cisomo ca Ambuye wathu cidacurukatu pamodzi ndi cikhulupiriro ndi cikondi ciri mwa Kristu Yesu.
15 Mauwa ali okhulupirika ndi oyenera konse kuti awalandire, kuti Kristu Yesu anadza ku dziko lapansi kupulumutsa ocimwa; wa iwowa ine ndine woposa;
16 komatu mwa ici anandicitira cifundo, kuti mwa ine, woyamba, Yesu Kristu akaonetsere kuleza mtima kwace konse kukhale citsanzo ca kwa iwo adzakhulupirira pa iye m'tsogolo kufikira moyo wosatha.
17 Ndipo kwa Mfumu yosatha, yosabvunda, yosaoneka, Mulungu wa yekha, ukhale ulemu ndi ulemerero, kufikira nthawi za nthawi. Amen.
18 Lamulo ili ndipereka kwa iwe, mwana wanga Timoteo, kuti, emonga mwa zonenera zidakutsogolera iwe kale, ulimbane nayo nkhondo yabwino;
19 ndi kukhala naco cikhulupiriro ndi cikumbu mtima cokoma, cimene ena adacikankha, cikhulupiriro cao cidatayika;
20 a iwo ali Humenayo ndi Alesandro, amene ndawapereka kwa Satana, kuti aphunzire kusalankhula zamwano.
1 Ndidandaulira tsono, poyambayamba, kuti acitike mapembedzo, mapemphero, mapembedzero, mayamiko, cifukwa ca anthu onse;
2 cifukwa ca mafumu ndi onse akucita ulamuliro kuti m'moyo mwathu tikakhale odika mtima, ndi acete m'kulemekeza Mulungu, ndi m'kulemekezeka monse.
3 Pakuti ici ncokoma ndi colandirika pamaso pa Mulungu Mpulumutsi wathu;
4 amene afuna anthu onse apulumuke, nafike pozindikira coonadi.
5 Pakuti pali Mulungu mmodzi, ndi Mtetezi mmodzi pakati pa Mulungu ndi anthu, ndiye munthu, Kristu Yesu,
6 amene anadzipereka yekha ciombolom'malo mwa onse; umboni m'nyengo zace;
7 umene anandiika ine mlaliki wace ndi mtumwi (ndinena zoona, wosanama ine), mphunzitsi wa amitundu m'cikhulupiriro ndi coonadi.
8 Cifukwa cace ndifuna kuti amunawo apemphere pamalo ponse, ndi kukweza manja oyera, opanda mkwiyo ndi makani.
9 Momwemonso, akazi adzibveke okha ndi cobvala coyenera, ndi manyazi, ndi cidziletso; osati ndi tsitsi lace loluka, ndi golidi kapena ngale, kapena maraya a mtengo wace wapatali;
10 komatu (umo mokomera akazi akubvomereza kulemekeza Mulungu), mwa nchito zabwino.
11 Mkazi aphunzire akhale wacete m'kumvera konse.
12 Koma sindilola ine kuti mkazi aphunzitse, kapena kulamulira mwamuna; komatu akhale cete.
13 Pakuti Adamu anayamba kulengedwa, pamenepo Heva;
14 ndipo Adamu sananyengedwa, koma mkaziyo ponyengedwa analowa m'kulakwa;
15 koma adzapulumutsidwa mwa kubala mwana, ngati akhala m'cikhulupiriro ndi cikondi ndi ciyeretso pamodzi ndi cidziletso.
1 Mauwa ali okhulupirika, ngati munthu akhumba udindo wa woyang'anira, aifuna nchito yabwino.
2 Ndipo kuyenera woyang'anira akhale wopanda cirema, mwamuna wa mkazi mmodzi, wodzisunga, wodziletsa, wolongosoka, wokonda kucereza alendo, wokhoza kuphunzitsa;
3 wosati woledzera, kapena womenyana ndeu; komatu wofatsa, wopanda ndeu, wosakhumba cuma;
4 woweruza bwino nyumba yace ya iye yekha, wakukhala nao ana ace omvera iye ndi kulemekezeka konse.
5 Koma ngati munthu sadziwa kuweruza nyumba ya iye yekha, adzasunga bwanji Mpingo wa Mulungu?
6 Asakhale wophunza, kuti podzitukumula ungamgwere mlandu wa mdierekezi.
7 Kuyeneranso kuti iwo akunja adzakhoza kumcitira umboni wabwino; kuti ungamgwere mtonzo, ndi msampha wa mdierekezi.
8 Momwemonso atumiki akhale olemekezeka, osanena pawiri, osamwetsa vinyo, osati a cisiriro conyansa;
9 okhala naco cinsinsi ca cikhulupiriro m'cikumbu mtima coona.
10 Koma iwonso ayambe ayesedwe; pamenepo atumikire, akakhala opanda cifukwa.
11 Momwemonso akazi akhale olemekezeka, osadierekeza, odzisunga, okhulupirika m'zonse.
12 Atumiki akhale mwamuna wa mkazi mmodzi, akuweruza bwino ana ao, ndi iwo a m'nyumba yao ya iwo okha.
13 Pakuti iwo akutumikira bwino adzitengera okha mbiri yabwino, ndi kulimbika kwakukuru m'cikhulupiriro ca mwa Kristu Yesu.
14 Izi ndikulembera ndi kuyembekeza kudza kwa iwe posacedwa, koma ngati ndicedwa,
15 kuti udziwe kuyenedwa kwace pokhala m'nyumba ya Mulungu, ndiye Eklesia wa Mulungu wamoyo, mzati ndi mcirikizo wa coonadi.
16 Ndipo pobvomerezeka, cinsinsi ca kucitira Mulungu ulemu ncacikuru: iye amene anaonekera m'thupi, anayesedwa wolungama mumzimu, anapenyeka ndi angelo, analalikidwa mwa amitundu, wokhulupiridwa m'dziko lapansi, wolandiridwa m'ulemerero.
1 Koma Mzimu anena monenetsa, kuti m'masiku otsiriza ena adzataya cikhulupiriro, ndi kusamala mizimu yosoceretsa ndi maphunziro a ziwanda,
2 m'maonekedwe onyenga a iwo onena mabodza, olocedwa m'cikumbu mtima mwao monga ndi citsulo camoto;
3 akuletsa ukwati, osivitsa zakudya zakuti, zimene Mulungu anazilenga kuti acikhulupiriro ndi ozindikira coonadi azilandire ndi ciyamiko.
4 Pakuti colengedwa conse ca Mulungu ncabwino, ndipo palibe kanthu kayenera kutayika, ngati kalandiridwa ndi ciyamiko;
5 pakuti kayeretsedwa ndi Mau a Mulungu ndi kupemphera.
6 Ngati ukumbutsa abale zinthu izi, udzakhala mtumiki wabwino wa Kristu Yesu, woleredwa m'mauwo a cikhulupiriro, ndi malangizo abwino amene udawatsata;
7 koma nkhani zacabe ndi za akazi okalamba ukane. Ndipo udzizoloweretse kucita cipembedzo;
8 pakuti cizolowezi ca thupi cipindula pang'ono, koma cipembedzo cipindula zonse, popeza cikhala nalo Lonjezano la ku moyo uno, ndi la moyo ulinkudza.
9 Okhulupirika mauwa ndi oyenera kulandiridwa konse.
10 Pakuti kukalingako tlgwiritsa nchito ndi kuyesetsa, cifukwa ciyembekezo cathu tiri naco pa Mulungu wamoyo, amene ali Mpulumutsi wa anthu onse, makamaka wa okhulupira.
11 Lamulira izi, nuziphunzitse.
12 Munthu asapeputse ubwana wako; komatu khala citsanzo kwa iwo okhulupira, m'mau, m'mayendedwe, m'cikondi, m'cikhulupiriro, m'kuyera mtima.
13 Kufikira ndidza ine, usamalire kuwerenga, kucenjeza, kulangiza.
14 Usanyalapse mphatsoyo iri mwa iwe, yopatsidwa kwa iwe mwa cinenero, pamodzi ndi kuika kwa manja a akulu.
15 Izi uzisamalitse; mu izi ukhale; kuti kukula mtima kwako kuonekere kwa onse.
16 Udzipenyerere wekha, ndi ciphunzitsoco. Uzikhala muizi; pakuti pocita ici udzadzipulumutsa iwe wekha ndi iwo akumva iwe.
1 Mkulu usamdzudzule, komatu umdandaulire ngati atate; anyamata ngati abale;
2 akazi akulu ngati amai; akazi ang'ono ngati alongo, m'kuyera mtima konse.
3 Citira ulemu amasiye amene ali amasiye ndithu.
4 Koma ngati wamasiye wina ali nao ana kapena adzukulu, ayambe aphunzire iwo kucitira ulemu a m'banja lao, ndi kubwezera akuwabala; pakuti ici ncolandirika pamaso pa Mulungu.
5 Koma iye amene ali wamasiye ndithu, nasiyidwa yekha, ayembekezera Mulungu, nakhalabe m'mapembedzo ndi mapemphero usiku ndi usana.
6 Koma iye wakutsata zomkondweretsa, adafa pokhala ali ndi moyo,
7 Ndipo izi ulamulire, kuti akhale opanda ciremao
8 Koma ngati wina sadzisungiratu mbumba yace ya iye yekha, makamaka iwo a m'banja lace, wakana cikhulupiriro iye, ndipo aipa koposa wosakhulupira.
9 Asawerengedwe wamasiye ngati sanafikire zaka makumi asanu ndi limodzi, atakhala mkazi wa mwamuna mmodzi,
10 wa mbiri ya nchito zabwino; ngati walera ana, ngati wacereza alendo, ngati adasambitsa mapazi a nzera mtima, ngati wathapdiza osautsidwa, ngati anatsatadi nchito zonse zabwino.
11 Koma amasiyeang'ono uwakane; pakuti pamene ayambakumcitira Kristu cipongwe afuna kukwatiwa;
12 pokhala naco citsutso, popeza adataya cikhulupiriro cao coyamba.
13 Ndipo aphunziraponso kucita ulesi, aderuderu; koma osati ulesi wokha, komatunso alankhula zopanda pace, nacita mwina ndi mwina, olankhula zosayenera.
14 Cifukwa cace nditi akwatiwe amasiye ang'ono, nabale ana, naweruzire nyumba, osapatsa cifukwa kwa mdaniyo cakulalatira;
15 pakuti adayamba enakupatuka ndi kutsata Satana.
16 Ngati mkazi wina wokhulupira ali nao amasiye, iye awathandize, ndipo Mpingowo usalemedwe; kuti uthandize iwo amene ali amasiye ndithu.
17 Akuru akuweruza bwino ayesedwe oyenera ulemu wowirikiza, makamaka iwo akucititsa m'mau ndi m'ciphunzitso.
18 Pakuti malembo ati, Usapunamiza ng'ombe yopuntha tirigu. Ndipo, Wogwira nchito ayenera kulipira kwace.
19 Pa mkulu usalandire comnenera, koma pakhale mboni ziwiri kapena zitatu.
20 Iwo akucimwa uwadzudzule pamaso pa onse, kuti otsalawo acite mantha.
21 Ndikucitira umboni pamaso pa Mulungu, ndi Kristu Yesu, ndi angelo osankhika, kuti usunge izi kopanda kusankhiratu, wosacita kanthu monga mwa tsankhu.
22 Usafulumira kuika manja pa munthu ali yense, kapena usayanjana nazo zoipa za eni; udzisunge wekha woyera mtima.
23 Usakhalenso wakumwa madzi okha, komatu ucite naye vinyo pang'ono, cifukwa ca mimba yako ndi zofoka zako zobwera kawiri kawiri.
24 Zocimwa za anthu ena ziri zooneka-kale, zitsogola kunka kumlandu; koma enanso ziwatsata.
25 Momwemonso pali nchito zokoma zinaonekera kale; ndipo zina zosati zotere sizikhoza kubisika.
1 Onse amene ali akapolo a m'goli, ayesere ambuye a iwo okha oyenera ulemu wonse, kuti dzina la Mulungu ndi ciphunzitso zisacitidwe mwano.
2 Ndipo iwo akukhala nao ambuye okhulupira, asawapeputse popeza ali abale; koma makamaka awatumikire popeza ali okhulupira ndi okondedwa, oyanjana nao pa cokomaco, Izi uphunzitse, nucenjeze.
3 Ngati munthu aphunzitsa zina, wosabvomerezana nao mau a moyowo a Ambuye wathu Yesu Kristu, ndi ciphunzitsoco ciri monga mwa cipembedzo:
4 iyeyo watukumuka, wosadziwa kanthu, koma ayarukira pa mafunso ndi makani a mau, kumene zieokerako njiru, ndeu, zamwano, mayerekezo oipa;
5 makani opanda pace a anthu oipsika nzeru ndi ocotseka coonadi, akuyesa kuti cipembedzo cipindulitsa.
6 Koma cipembedzo pamodzi ndi kudekha cipindulitsa kwakukuru;
7 pakuti sitinatenga kanthu polowa m'dziko lapansi, ndiponso sitikhoza kupita nako kanthu pocoka pano;
8 koma pokhala nazo zakudya ndizopfunda, zimenezi zitikwanire.
9 Koma iwo akufuna kukhala acuma amagwa m'ciyesero ndi m'msampha, ndi m'zilakolako zambiri zopusa ndi zopweteka, zotere zonga zimiza anthu m'cionongekondi citayiko.
10 Pakuti muzu wa zoipa zonse ndiwo cikondi ca pa ndalama; cimene ena pocikhumba, anasocera, nataya cikhulupiriro, nadzipyoza ndi zowawa zambiri.
11 Koma iwe, munthu wa Mulungu iwe, thawa izi; nutsate cilungamo, cipembedzo, cikhulupiriro, cikondi, cipiriro, cifatso.
12 Limba nayo nkhondo yabwino ya cikhulupiriro, gwira moyo wosatha, umene adakuitanira, ndipo wabvomereza cibvomerezo cabwino pamaso pa mboni zambiri.
13 Ndikulamulira pamaso pa Mulungu, wozipatsa zinthu zonse moyo, ndi Kristu Yesu, amene anacitira umboni cibvomerezo cabwino kwa Pontiyo Pilato;
14 kuti usunge lamulolo, lopanda banga, lopanda cirema, kufikira maonekedwe a Ambuye wathu Yesu Kristu;
15 limene adzalionetsa m'nyengo za iye yekha, amene ali Mwini Mphamvu wodala ndi wayekha, ndiye Mfumu ya mafumu ndi Mbuye wa ambuye;
16 amene iye yekha ali nao moyo wosatha, wakukhala m'kuunika kosakhozeka kufikako; amene munthu sanamuona, kapena sakhoza kumuona; kwa iye kukhale ulemu ndi mphamvu yosatha. Amen.
17 Lamulira iwo acuma m'nthawi yino ya pansi pano, kuti asadzikuze, kapena asayembekezere cuma cosadziwika kukhala kwace, koma Mulungu, amene atipatsa ife zonse kocurukira, kuti tikondwere nazo;
18 kuti acite zabwino, naeuruke ndi nchito zabwino, nakondwere kugawira ena, nayanjane;
19 nadzikundikire okha maziko okoma ku nyengo ikudzayi, kuti akagwire moyo weni weniwo.
20 Timoteo iwe, dikira cokusungitsa, ndi kulewa zokamba zopanda pace ndi zotsutsana za ici cichedwa cizindikiritso konama;
21 cimene ena pocibvomereza 1 adalakwa ndi kutaya cikhulupiriro. Cisomo cikhale nanu.