1

1 AWA ndi mau amene Mose ananena kwa Israyeli wonse, tsidya la Yordano m'cipululu, m'cidikha ca pandunji pa Sufu, pakati pa Parani, ndi Tofeli, ndi Labani, ndi Hazeroti, ndi Di Zahabi.

2 Ulendo wace wocokera ku Horebe wofikira ku Kadesi Barinea, wodzera njira ya phiri la Seiri, ndiwo wa masiku khumi ndi limodzi.

3 Ndipo kunali, caka ca makumi anai, mwezi wakhumi ndi umodzi, tsiku loyamba la mweziwo, Mose ananena ndi ana a Israyeli, monga mwa zonse Yehova adamlamulira awauze;

4 atakantha Sihoni mfumu ya Aamori, wakukhala m'Hesiboni, ndi Ogi mfumu ya Basana, wakukhala m'Asitaroti, ku Edrei.

5 Tsidya lija la Yordano, m'dziko la Moabu, Mose anayamba kufotokozera cilamulo ici, ndi kuti.

6 Yehova Mulungu wathu ananena ndi ife m'Horebe, ndi kuti, Yakwanira nthawi yokhala inu m'phiri muno;

7 bwererani, yendani ulendo wanu ndi kumuka ku mapiri a Aamori, ndi koyandikizana nao, kucidikha, kumapiri, ndi kunsi ndi kumwela, ndi kumphepete kwa nyanja, dziko la Akanani, ndi Lebano, kufikira nyanja yaikuru Firate.

8 Taonani, ndakupatsani dzikoli pamaso panu, lowani landirani dziko limene Yehova analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isake, ndi Yakobo, kuti ili ndidzawapatsa iwo ndi mbeu zao pambuyo pao.

9 Ndipo muja ndinanena ndi inu, ndi kuti, Sinditha ine kukunyamulani ndekha;

10 Yehova Mulungu wanu anakucurukitsani, ndipo taonani, lero mucuruka ngati nyenyezi za kumwamba.

11 Yehova Mulungu wa makolo anu, acurukitsire ciwerengero canu calero ndi cikwi cimodzi, nakudalitseni monga iye ananena nanu!

12 Ndikasenza bwanji ndekha kupsinya kwanu, ndi katundu wanu, ndi kulimbana kwanu?

13 Dzifunireni amuna anzeru, ndi ozindikira bwino, ndi odziwika mwa mafuko anu, ndipo ndidzawaika akhale akuru anu.

14 Pamenepo munandiyankha ndi kuti, Mau mwanenawa ndi abwino kuwacita.

15 Potero ndinatenga akuru a mapfuko anu, amuna anzeru, ndi odziwika, ndi kuwaika akhale akuru anu, atsogoleri a zikwi, ndi atsogoleri a mazana, ndi atsogoleri a makumi asanu, ndi atsogoleri a makumi, ndi akapitao, a mapfuko anu.

16 Ndipo ndinauza oweruza anu muja, ndi kuti, Mverani milandu ya pakati pa abale anu, ndi kuweruza kolungama pakati pa munthu ndi mbale wace, ndi mlendo wokhala naye.

17 Musamasamalira munthu poweruza mlandu; ang'ono ndi akuru muwamvere m'modzimodzi; musamaopa nkhope ya munthu; popeza ciweruzo nca Mulungu; ndipo mlandu ukakulakani mubwere nao kwa ine, ndidzaumva.

18 Ndipo ndinakuuzani muja zonse muyenera kuzicita.

19 Pamenepo tinayenda ulendo kucokera ku Horebe, ndi kubzyola m'cipululu cacikuru ndi coopsa ciija conse munacionaci, pa njira ya ku mapiri a Aamori, monga Yehova Mulungu wathu anatiuza; ndipo tinadza ku Kadesi Barinea.

20 Ndipo ndinati kwa inu, Mwafikira mapiri a Aamori, amene Yehova Mulungu wathu atipatsa.

21 Taonani, Yehova Mulungu wanu wapatsa dzikoli pamaso panu; kwerakoni, landirani, monga Yehova Mulungu wa makolo anu, wanena ndi inu; musamacita mantha, musamatenga nkhawa.

22 Ndipo munayandikiza kwa ine inu nonse, ndi kuti, Titumize amuna atitsogolere, kuti akatizondere dziko ndi kutibwezera mau akunena za njira ya kukwera nayo ife pomka komweko, ndi za midzi yoti tidzafikako.

23 Ndipo cinandikomera cinthu ici; ndipo ndinatenga amuna khumi ndi awiri ainu, pfuko limodzi mwamuna mmodzi;

24 amenewa anatembenuka nakwera kumapiri nalowa ku cigwa ca Esikolo, nacizonda.

25 Ndipo anatengako zipatso za dzikoli m'manja mwao, natsikira nazo kwa ife, natibwezera mau ndi kuti, Dzikoli Yehova Mulungu wathu atipatsa ndi labwino.

26 Koma simunafuna kukwerako, ndipo munapikisana nao mau a Yehova Mulungu wanu.

27 Ndipo munadandaula m'mahema mwanu, ndi kuti, Popeza anatida Yehova, iye anatiturutsa m'dziko la Aigupto, kutipereka m'manja mwa Aamori, ationonge.

28 Tikwere kuti? abale athu atimyukitsa mitima yathu, ndi kuti, Anthuwo ndiwo akulu ndi atali akuposa ife; midzi ndi yaikulu ndi ya malinga ofikira m'mwamba: tinaonakonso ana a Anaki.

29 Pamenepo ndinati kwa inu, Musamaopsedwa, musamacita mantha nao.

30 Yehova Mulungu wanu wakutsogolera inu, iye adzathirira inu nkhondo, monga mwa zonse anakucitirani m'Aigupto pamaso panu;

31 ndi kucipululu, kumene munapenya kuti Yehova Mulungu wanu anakunyamulani, monga anyamula mwana wace wamwamuna, m'njira monse munayendamo, kufikira mutalowa m'malo muno.

32 Koma m'cinthu ici simunakhulupirira Yehova Mulungu wanu,

33 amene anakutsogolerani m'njira, kukufunirani malo akumanga mahema anu ndi mota usiku, kukuonetserani njira yoyendamo inu, ndi mumtambo usana.

34 Ndipo Yehova anamva mau a kunena kwanu, nakwiya, nalumbira, ndi kuti,

35 Palibe mmodzi wa anthu awa a mbadwo uno woipa adzaona dziko lokomalo ndinalumbira kupatsa makolo anuli.

36 Koma Kalebi mwana wa Yefune, iye adzaliona; ndidzampatsa iye dziko limene anapondapo, ndi ana ace; popeza analimbika ndi kutsata Yehova.

37 Yehova anakwiya ndi inenso cifukwa ca inu, ndi kuti, lwenso sudzalowamo.

38 Yoswa mwana wa Nuni, wakuima pamaso pako, iye adzalowamo; umlimbitse mtima; popeza iye adzalandiritsa Israyeli.

39 Ndipo ana anu amene mudanena, Adzakhala ogulidwa, ndi ana anu osadziwa cabwino kapena coipa ndi pano, iwo adzalowamo, ndidzawapatsa iwo ili, adzalilandira ndi iwo.

40 Koma inu, bwererani, mukani ulendo wanu kucipululu, njira ya ku Nyanja Yofiira.

41 Pamenepo munayankha ndi kunena ndi ine, Tacimwira Yehova, tidzakwera ndi kuthira mkhondo monga mwa zonse Yehova Mulungu wathu atiuza. Ndipo munadzimangira munthu yense zida zace za nkhondo, nimunakonzeka kukwera kumka kumapiri.

42 Koma Yehova anati kwa ine, Nena nao, Musakwerako, kapena kuthira nkhondo; popeza sindiri pakati panu; angakukantheni adani anu.

43 Pamene ndinanena ndi inu simunamvera; koma munatsutsana nao mau a Yehova ndi kucita modzikuza, nimunakwera kumka kumapiri.

44 Ndipo Aamori, akukhala m'mapiri muja, anaturuka kukomana ndi inu, nakupitikitsani, monga zimacita njuci, nakukanthani m'Seiri, kufikira ku Horima.

45 Ndipo munabwerera ndi kulira pamaso pa Yehova; koma Yehova sanamvera mau anu, kapena kukucherani khutu.

46 Potero munakhala m'Kadesi masiku ambiri, monga mwa masiku munakhalako.

2

1 Pamenepo tinabwerera, ndi kuyenda kumka kucipululu, kutsata njira ya Nyanja Yofiira, monga Yehova adanena ndi ine; ndipo tinapaza phiri la Seiri masiku ambiri.

2 Ndipo Yehova ananena ndi ine, ndi kuti,

3 Yakwanira nthawi yakupaza inu phiri ili; tembenukani kumka kumpoto,

4 Ndipo uuze anthu, ndi kuti, Mukapite kubzyola malire a abale anu, ana a Bsau okhala m'Seiri; ndipo adzakuopani; mucenjere ndithu;

5 musalimbana nao; popeza sindikupatsakoni dziko lao, pangakhale popondapo phazi lanu ai pakuti ndapatsa Bsau phiri la Seiri likhale lace lace.

6 Mugulane nao cakudya ndi ndarama, kuti mudye; mugulane naonso madzi kuti mumwe.

7 Pakuti Yehova Mulungu wanu anakudalitsani mu nchito zonse za manja anu; anadziwa kuyenda kwanu m'cipululu ici cacikuru; zaka izi makumi anai Yehova Mulungu wanu anakhala ndi inu; simunasowa kanthu.

8 Potero tinapitirira abale athu, ana a Bsau okhala m'Seiri, njira ya cidikha, ku Elati ndi ku Ezioni Geberi.

9 Pamenepo tinatembenuka ndi kudzera njira ya cipululu ca Moabu. Ndipo Yehova anati kwa ine, Usabvuta Moabu, kapena kuutsana naye nkhondo; popeza sindidzakupatsako dziko lace likhale lako lako; pakuti ndinapatsa ana a Loti Ari likhale lao lao.

10 (Aemi anakhalamo kale, ndiwo anthu akuru, ndi ambiri, ndi atalitali, ngati Aanaki.

11 Anawayesa iwonso Arefai, monga Aanaki; koma Amoabu awacha Aemi.

12 Ndipo Ahori anakhala m'Seiri kale, koma ana a Esau analanda dziko lao, nawaononga pamaso pao, nakhala m'malo mwao; monga Israyeli anacitira dziko lace lace, limene Yehova anampatsa.)

13 Ukani tsopano, olokani mtsinje wa Zeredi. Ndipo tinaoloka mtsinje wa Zeredi.

14 Ndipo masiku amene tinayenda kucokera ku Kadesi Barinea, kufikira tidaoloka mtsinje wa Zeredi, ndiwo zaka makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu; kufikira utatha mbadwo wonse wa amuna ankhondo m'cigono, monga Yehova adawalumbirira.

15 Komanso dzanja la Yehova linatsutsana nao, kuwaononga m'cigono, kufikira adawatha.

16 Ndipo kunali, atatha kufa amuna onse ankhondo mwa anthu,

17 Yehova ananena ndi ine, ndi kuti,

18 Lero lomwe utumphe malire a Moabu, ndiwo Ari.

19 Ndipo pamene uyandikiza popenyana ndi ana a Amoni, usawabvuta, kapena kuutsana nao; popeza sindidzakupatsako dziko la ana a Amoni likhale lako lako; popeza ndinapatsa ana a Loti ili likhale lao lao.

20 (Ilinso aliyesa dziko la Arefai; Arefai anakhalamo kale; koma Aamoni awacha Azamzumi;

21 ndiwo anthu akuru, ndi ambiri, ndi atalitali, monga Aanaki; koma Yehova anawaononga pamaso pao; ndipo analanda dziko lao, nakhala m'malo mwao;

22 monga iye anacitira ana a Bsau, akukhala m'Seiri, pamene anaononga Ahori pamaso pao; ndipo analanda dziko lao, nakhala m'malo mwao kufikira lero lomwe.

23 Kunena za Aavi akukhala m'midzi kufikira ku Gaza, Akafitori, akufuma ku Kafitori, anawaononga, nakhala m'malo mwao.)

24 Uka, yenda ulendo wako, ndi kuoloka mtsinje wa Arinoni; taonani, ndapereka Sihoni mfumu ya Hesiboni, M-amori, ndi dziko lace m'dzanja lako; yamba kulilandira, ndi kuutsana naye nkhondo.

25 Tsiku lino ndiyamba kuopsetsa nawe ndi kucititsa mantha nawe anthu a pansi pa thambo lonse, amene adzamva mbiri yako, nadzanjenjemera, nadzawawidwa cifukwa ca iwe.

26 Ndipo ndinatuma amithenga ocokera ku cipululu ca Kedemoti kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni ndi mau a mtendere, ndi kuti,

27 Ndipitire m'dziko mwako; ndidzatsata mseu, osapatuka ine ku dzanja lamanja kapena kulamanzere,

28 Undigulitse cakudya ndi ndarama, kuti ndidye; ndi kundipatsa madzi kwa ndarama, kuti ndimwe; cokhaci ndipitire coyenda pansi;

29 monga anandicitira ana a Esau akukhala m'Seiri, ndi Amoabu akukhala m'Ari; kufikira nditaoloka Yordano kulowa dziko limene Yehova Mulungu wathu atipatsa.

30 Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanatilola kupitira kwao; popeza Yehova Mulungu wanu anaumitsa mzimu wace, nalimbitsa mtima wace, kuti ampereke m'dzanja lanu, monga lero lino.

31 Ndipo Yehova anati kwa ine, Taona, ndayamba kupereka Sihoni ndi dziko lace pamaso pako; yamba kulandira dziko lace likhale lako lako.

32 Pamenepo Sihoni anaturuka kukomana nafe, iye ndi anthu ace onse, kugwirana nafe nkhondo ku Yahaza.

33 Ndipo Yehova Mulungu wathu anampereka iye pamaso pathu; ndipo tinamkantha, iye ndi ana ace amuna ndi anthu ace onse.

34 Ndipo muja tinalanda midzi yace yonse; ndipo tinaononga konse midzi yonse, amuna ndi akazi ndi ana; sitinasiyapo ndi mmodzi yense.

35 Zoweta zokha tinadzifunkhira, pamodzi ndi zofunkha za midzi tidailanda.

36 Kuyambira ku Aroeri, ndiko kumphepete kwa mtsinje wa Arinoni, ndi ku mudzi wokhala kumtsinje kufikira ku Gileadi, kunalibe mudzi wakutitalikira malinga ace; Yehova Mulungu wathu anapereka yonse pamaso pathu.

37 Ku dziko la ana a Amoni lokha simunayandikiza; dera lonse la mtsinje wa Yaboki, ndi midzi ya kumapiri, ndi kwina kuli konse Yehova Mulungu wathu anatiletsa.

3

1 Pamenepo tinatembenuka, ndi kubwera kumka njira ya ku Basana; ndipo Ogi mfumu ya Basana anaturuka kukomana nafe, kugwirana nafe nkhondo, iye ndi anthu ace onse, ku Edrei.

2 Ndipo Yehova anati kwa ine, Usamuopa; popeza ndampereka iye ndi anthu ace onse, ndi dziko lace, m'dzanja lako; umcitire monga umo unacitira Sihoni mfumu ya Aamori, amene anakhala m'Hesiboni.

3 Potero Yehova Mulungu wathu anaperekanso m'manja mwathu Ogi mfumu ya Basana, ndi anthu ace onse, ndipo tinamkantha kufikira sanamtsalira ndi mmodzi yense.

4 Ndipo muja tinalanda midzi yace yonse; kunalibe mudzi sitinaulanda m'manja mwao, midzi makumi asanu ndi limodzi, dera lonse la Arigobi, dziko la Ogi m'Basana.

5 Yonseyi ndiyo midzi yozinga ndi malinga atali, zitseko, ndi mipiringidzo; pamodzi ndi midzi yambirimbiri yopanda malinga.

6 Ndipo tinaiononga konse, monga umo tinacitira Sihoni mfumu ya Hesiboni, ndi kuononga konse midzi yonse, amuna, akazi ndi ana.

7 Koma zoweta zonse ndi zofunkha za m'midzi, tinadzifunkhira tokha.

8 Ndipo muja tinalanda dziko m'manja mwa mafumu awiri a Aamori okhala tsidya lija la Yordano, kuyambira mtsinje wa Arinoni kufikira phiri la Herimoni;

9 (Asidoni alicha Herimoni Sirioni, koma Aamori alicha Seniri);

10 midzi yonse ya kucidikha, ndi Gileadi lonse, ndi Basana lonse kufikira ku Saleka ndi Edrei, midzi ya dziko la Ogi m'Basana.

11 (Pakuti Ogi mfumu ya Basana anatsala yekha wa iwo otsalira Arefai; taonani, kama wace ndiye kama wacitsulo; sukhala kodi m'Raba wa ana a Amoni? utali wace mikono isanu ndi inai, kupingasa kwace mikono inai, kuyesa mkono wa munthu.)

12 Ndipo dziko ili tinalilanda muja; kuyambira ku Aroeri, wa ku mtsinje wa Arinoni, ndi dera lina la ku mapiri a Gileadi, ndi midzi yace, ndinapatsa Arubeni ndi Agadi.

13 Ndi cotsalira ca Gileadi, ndi Basana lonse, dziko la Ogi, ndinapatsa pfuko la hafu la Manase; dziko lonse la Arigobi, pamodzi ndi Basana. (Ndilo lochedwa dziko la Arefai.

14 Yairi mwana wa Manase analanda dziko lonse la Arigobi, kufikira malire a Agesuri ndi Amaakati; nalicha dzina lace, Basana Haroti Yairi, kufikira lero lino.)

15 Ndipo ndinampatsa Makiri Gileadi.

16 Koma ndinapatsa Arubeni ndi Agadi kuyambira ku Gileadi kufikira ku mtsinje wa Arinoni, pakati pa cigwa ndi malire ace, kufikira mtsinje wa Yaboki, ndiwo malire a ana a Amoni;

17 ndi cidikha, ndi Yordano ndi malire ace, kuyambira ku Kinerete kufikira ku nyanja ya kucidikha, ndiyo Nyanja ya Mcere, patsinde pa Pisiga, kum'mawa.

18 Ndipo ndinauza inu muja, ndi kuti, Yehova Mulungu wanu wakupatsani dziko ili likhale lanu lanu, muoloke, amuna onse amphamvu obvala zida zao, pamaso pa abale anu ana a Israyeli.

19 Koma akazi anu, ndi ana anu, ndi zoweta zanu, (ndidziwa muli nazo zoweta zambiri), zikhale m'midzi yanu imene ndinakupatsani;

20 kufikira Yehova atapumulitsa abale anu, monga anapumulitsa inu, nalandira iwonso dziko limene Yehova Mulungu wanu awapatsa tsidya lila la Yordano; pamenepo mudzabwerera munthu yense ku colowa cace, cimene ndinakupatsani.

21 Ndipo ndinauza Yoswa muja, ndi kuti, Maso ako anapenya zonse Yehova Mulungu wanu anawacitira mafumu awa awiri; momwemo Yehova adzacitira maufumu onse kumene muolokerako.

22 Musawaopa popeza Yehova Mulungu wanu, ndiye agwirira inu nkhondo.

23 Ndipo ndinapempha cifundo kwa Yehova nthawi yomwe ija, ndi kuti,

24 Ambuye Yehova, mwayamba Inu kuonetsera mtumiki wanu ukulu wanu, ndi dzanja lanu lamphamvu; pakuti Mulungu ndani m'mwamba kapena pa dziko lapansi wakucita monga mwa nchito zanu, ndi monga mwa mphamvu zanu?

25 Ndioloketu, ndilione dziko lokomali liri tsidya la Yordano, mapiri okoma aja, ndi Lebano.

26 Koma Yehova anakwiya ndi ine, cifukwa ca inu, sanandimvera ine; ndipo Yehova anati kwa ine, Cikukwanire, usaonjezenso kunena ndi Ine za cinthuci.

27 Kwera kumwamba ku Pisiga, nukweze maso ako kumadzulo, ndi kumpoto, ndi kumwela, ndi kum'mawa, nuyang'ane ndi maso ako; popeza sudzaoloka Yordano uyo.

28 Koma langiza Yoswa, dioloketu numlimbitse mtima, ndi kumkhwimitsa, pakuti adzaoloka pamaso pa anthu awa, nadzawalandiritsa dziko ulionali likhale lao lao.

29 Potero tinakhala m'cigwamo pandunji pa Beti Peori.

4

1 Ndipo tsopano, Israyeli, dioloketu tamverani malemba ndi maweruzo, amene ndikuphunzitsani muwacite; kuti mukhale ndi moyo, ndi kulowa, ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akupatsani.

2 Musamaonjeza pa mau amene ndikuuzani, kapena kucotsapo, kuti musunge malamulo a Yehova Mulungu wanu, amene ndikuuzani.

3 Maso anu anapenya cocita Yehova cifuwa ca Baala Peori; pakuti amuna onse amene anatsata Baala Peori, Yehova Mulungu wanu anawaononga pakati panu.

4 Koma inu amene munamamatira Yehova Mulungu wanu muli ndi moyo nonsenu lero lomwe.

5 Taonani, ndinakuphunzitsani malemba ndi maweruzo, monga Yehova Mulungu wanga anandiuza ine, kuti muzicita cotero pakati pa dziko limene mumkako kulilandira likhale lanu Lanu.

6 Cifukwa cace asungeni, aciteni; pakuti ici ndi nzeru zanu ndi cidziwitso canu pamaso pa mitundu ya anthu akumva malemba ndi kuti, Ndithu mtundu waukuru uwu, ndiwo anthu anzeru ndi akuzindikira.

7 Pakuti dioloketu mtundu waukuru wa anthu ndi uti, wakukhala ndi Mulungu pafupi pao monga amakhala Yehova Mulungu wathu, pamene pali ponse timaitanira iye?

8 Ndipo mtundu waukuru wa anthu ndi uti, wakukhala nao malemba ndi maweruzo olungama, akunga cilamulo ici conse ndiciika pamaso panu lero lino?

9 Cokhaci, dzicenjerani nokha, ndi kusunga moyo wanu mwacangu, kuti mungaiwale zinthuzi adaziona maso anu, ndi kuti zisacoke kumtima kwanu masiku onse a moyo wanu; koma muzidziwitsa ana anu ndi zidzukulu zanu.

10 Tsikuli munaima pamaso pa Yehova Mulungu wanu m'Horebe muja Yehova anati kwa ine, Ndisonkhanitsire anthu, ndidzawamvetsa mau anga, kuti aphunzire kundiopa Ine masiku ao onse akukhala ndi moyo pa dziko lapansi, ndi kuti aphunzitse ana ao.

11 Ndipo munayandikiza ndi kuima patsinde pa phiri; ndi phizilo linayaka mota kufikira pakati pa thambo; kunali mdima, ndi mtambo, inde mdima bii.

12 Pamenepo Yehova ananena ndi inu ali pakati pa moto; munamva kunena kwa mau, osaona maonekedwe, koma kunenako.

13 Pamenepo anakufotokozerani cipangano cace, cimene anakulamulirani kucicita, ndiwo Mau Khumi; nawalemba pa magome awiri amiyala.

14 Ndipo Yehova anandilamulira muja ndikuphunzitseni malemba ndi maweruzo, kuti mukawacite m'dziko limene muolokerako kulilandira likhale lanu lanu.

15 Potero dzicenjerani nao moyo wanu ndithu; popeza simunapenya mafanidwe konse tsikuli Yehova ananena ndi inu m'Horebe, ali pakati pa moto;

16 kuti mungadziipse, ndi kudzipangira fano losema, lakunga cifaniziro ciri conse, mafanidwe a mwamuna kapena mkazi;

17 mafanidwe a nyama iri yonse iri pa dziko lapansi, mafanidwe a mbalame iri yonse yamapiko yakuuluka m'mlengalenga,

18 mafanidwe a cinthu ciri conse cokwawa pansi, mafanidwe a nsomba iri yonse yokhala m'madzi pansi pa dziko;

19 ndi kuti mungakweze maso anu kupenya kumwamba, ndipo poona dzuwa ndi mwezi ndi nyenyezi, khamu lonse la kumwamba, munganyengedwe ndi kuzigwadira, ndi kuzitumikira, zimene Yehova Mulungu wanu anagawira mitundu yonse ya anthu pansi pa thambo lonse.

20 Koma Yehova anakutengani, nakuturutsani m'ng'anjo yamoto, m'Aigupto, mukhale kwa iye anthu a colowa cace, monga mukhala lero lino.

21 Yehova anakwiyanso nane cifukwa ca mau anu, nalumbira kuti sindidzaoloka Yordano ine, ndi kuti sindidzalowa m'dziko lokomali Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colowa canu;

22 pakuti ndidzafa m'dziko muno, osaoloka Yordano; koma inu mudzaoloka, ndi kulandira dziko ili lokoma likhale lanu lanu.

23 Dzicenjerani, mungaiwale cipangano ca Yehova Mulungu wanu, cimene anapangana nanu, ndi kuti mungadzipangire fano losema, cifaniziro ca kanthu kali konse Yehova Mulungu wanu anakuletsani.

24 Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye moto wonyeketsa, ndi Mulungu wansanje.

25 Mutakabala ana, ndi zidzukulu, ndipo mutakakhala nthawi yaikuru m'dzikomo, ndi kudziipsa, ndi kupanga fano losema, m'cifaniziro ca kanthu kali konse, ndi kucita coipa pamaso pa Yehova, kuutsa mkwiyo wace:

26 ndiitana kumwamba ndi dziko lapansi zicite mboni pa inu lero lino, kuti mudzaonongeka msangatu kucotsedwa ku dziko limene muolokera Yordano kulilandira likhale lanu lanu; masiku anu sadzacuruka pamenepo, koma mudzaonongeka konse.

27 Ndipo Yehova adzakubalalitsani mwa mitundu ya anthu, nimudzatsala pang'ono mwa amitundu, kumene Yehova adzakutsogolerani kwao.

28 Ndipo kumeneko mudzatumikira milungu, nchito ya manja a anthu, mtengo ndi mwala, yosapenya, kapena kumva, kapena kudya, kapena kununkhiza.

29 Koma mukafuna Yehova Mulungu wanu kumeneko, mudzampeza, ngati mumfunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.

30 Mukakhala nao msauko, zikakugwerani zonsezi, masiku otsiriza mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumvera mau ace;

31 popeza Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu wacifundo; sadzakusiyani, kapena kukuonongani, kapena kuiwala cipangano ca makolo anu cimene analumbirira iwo.

32 Pakuti, funsiranitu, masiku adapitawo, musanakhale inu, kuyambira tsikuli Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi, ndi kuyambira malekezero ena a thambo kufikira malekezero anzace a thambo, ngati cinthu cacikuru conga ici cinamveka, kapena kucitika?

33 Kodi pali mtundu wa anthu udamva a Malungu akunena pakati pa moto, monga mudamva inu, ndi kukhala ndi moyo?

34 Kapena kodi anayesa Mulungu kumuka ndi kudzitengera mtundu mwa mtundu wina wa anthu, ndi mayesero, ndi zizindikilo, ndi zozizwa, ndi nkhondo, ndi mwa dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka, ndi mwa zoopsa zazikuru, monga mwa zonse Yehova Mulungu wanu anakucitirani m'Aigupto pamaso panu?

35 Inu munaciona ici, kuti mudziwe kuti Yehova ndiye Mulungu; palibe wina wopanda iye.

36 Anakumvetsani mau ace kucokera kumwamba, kuti akuphunzitseni; ndipo pa dziko lapansi anakuonetsani moto wace waukuru; nimunamva mau ace pakati pa moto.

37 Ndipo popeza anakonda makolo anu, anasankha mbeu zao zakuwatsata, nakuturutsani pamaso pace ndi mphamvu yace yaikuru, m'Aigupto;

38 kupitikitsa amitundu akuru ndi amphamvu oposa inu pamaso panu, kukulowetsani ndi kukupatsani dziko lao likhale colowa canu, monga lero lino.

39 Potero dziwani lero tino nimukumbukire m'mtima mwanu, kuti Yehova ndiye Mulungu, m'thambo la kumwamba ndi pa dziko lapansi; palibe wina.

40 Muzisunga malemba ace, ndi malamulo ace, amene ndikuzuzani lero lino, kuti cikukomereni inu ndi ana anu akukutsatani, ndi kuti masiku anu acuruke pa dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanu kosatha.

41 Pamenepo Mose anapatula midzi itatu tsidya lija la Yordano loturuka dzuwa;

42 kuti athawireko wakupha munthu, osamupha mnansi wace dala, osamkwiyira ndi kale lonse; ndi kuti, akathawira ku umodzi wa midzi iyi, akhale ndi moyo:

43 ndiyo Bezere, m'cipululu, m'dziko lacidikha, ndiwo wa Anrubeni; ndi Ramoti m'Gileadi, ndiwo wa Agadi; ndi Golani, m'Basana, ndiwo wa Amanase.

44 Ndipo ici ndi cilamulo Mose anaciika pamaso pa ana a Israyeli;

45 izi ndi mboni, ndi malemba, ndi maweruzo, Mose anazinena kwa ana a Israyeli, poturuka iwo m'Aigupto;

46 tsidya lija la Yordano, m'cigwa ca pandunji pa Beti Peori, m'dziko la Sihoni mfumu ya Aamori, wakukhala m'Hesiboni, amene Mose ndi ana a Israyeli anamkantha, poturuka iwo m'Aigupto;

47 ndipo analanda dziko lace, ndi dziko la Ogi mfumu ya Basana, mafumu awiri a Aamori, akukhala tsidya lija la Yordano loturuka dzuwa;

48 kuyambira ku Aroeri, ndiwo m'mphepete mwa mtsinje wa Arinoni, kufikira phiri la Sioni (ndilo Herimoni),

49 ndi cidikha conse tsidya lija la Yordana kum'mawa, kufikira nyanja ya kucidikha, pa tsinde lace la Pisiga.

5

1 Ndipo Mose anaitana Israyeli wonse, nanena nao, Tamverani, Israyeli, malemba ndi maweruzo ndinenawa m'makutu mwanu lero, kuti muwaphunzire, ndi kusamalira kuwacita.

2 Yehova Mulungu wathu anapangana nafe cipangano m'Horebe.

3 Yehova sanacita cipangano ici ndi makolo athu, koma ndi ife, ife amene tiri ndi moyo tonsefe pane lero.

4 Yehova ananena ndi inu popenyana maso m'phirimo, ali pakati pa moto,

5 (ndinalinkufma pakati pa Yehova ndi inu muja, kukulalikirani mau a Yehova; popeza munacita mantha cifukwa ca moto, osakwera m'phirimo) ndi kuti:

6 Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakuturutsa m'dziko la Aigupto, m'nyumba ya akapolo.

7 Usakhale nayo milungu yina koma Ine ndekha.

8 Usadzipangire iwe wekha fano losema, kapena cifaniziro ciri conse ca zinthu za m'thambo la kumwamba, kapena za m'dziko lapansi, kapena za m'madzi a pansi pa dziko;

9 usazipembedzere izo, usazitumikire izo; cifukwa Ine Yehova Mulungu wako ndine Mulungu wansanje, wakulanga ana cifukwa ca atate wao, kufikira mbadwo wacitatu ndi wacinai wa iwo amene akudana ndi Ine;

10 ndi kucitira cifundo anthu zikwi, a iwo amene akondana ndi Ine nasunga malamulo anga.

11 Usaehuledzinala Yehova Mulungu wako pacabe; cifukwa Yehova sadzamuyesa iye wosacimwa amene achula pacabe dzina lacelo.

12 Samalira tsiku la Sabata likhale lopatulika, monga Yehova Mulungu wako anakulamulira.

13 Masiku asanu ndi limodzi uzigwiritsa nchito, ndi kucita nchito zako zonse;

14 koma tsiku lacisanu ndi ciwiri ndilo Sabata la Yehova Mulungu wako; usamagwira nchito iri yonse, iwe, kapena mwana wako wamwamuna, kapena mwana wako wamkazi, kapena wanchito wako wamwamuna, kapena wanchito wako wamkazi, kapena ng'ombe yako, kapena buru wako, kapena zoweta zako ziri zonse, kapena mlendo wokhala m'mudzi mwako; kuti wanchito wako wamwamuna ndi wanchito wako wamkazi apumule monga iwe mwini.

15 Ndipo uzikumbukilakuti unali kapolo m'dziko la Aigupto, ndi kuti Yehova Mulungu wako anakuturutsako ndi dzanja lamphamvu ndi mkono wotambasuka; cifukwa cace Yehova Mulungu wako anakulamulira kusunga tsiku la Sabata.

16 Lemekeza atate wako ndi amako, monga Yehova Mulungu wako anakulamulira; kuti masiku ako acuruke, ndi kuti cikukomere, m'dziko limene Yehova Mulungu wako akupatsa iwe.

17 Usaphe.

18 Usacite cigololo.

19 Usabe.

20 Usamnamizire mnzako.

21 Usasirire mkazi wace wa mnzako; usakhumbe nyumba yace ya mnzako, munda wace, kapena wanchito wace wamwamuna, kapena wanchito wace wamkazi, ng'ombe yace, kapena buru wace, kapena kanthu kali konse ka mnzako.

22 Yehova ananena mau awa kwa msonkhano wanu wonse, m'phirimo ali pakati pa moto, pamtambo, pamdima bii, ndi mau akuru; osaonjezapo kanthu. Ndipo anawalembera pa magome awiri amiyala, nandipatsa awa.

23 Ndipo kunali, pamene munamva liu loturuka pakati pa mdima, potentha phiri ndi moto, munayandikiza kwa ine, ndiwo mafumu onse a mapfuko anu ndi akuru anu;

24 ndipo munati, Taonani, Yehova Mulungu wathu anationetsa ulemerero wace, ndi ukuru wace, ndipo tidamva liu lace ali pakati pa mote; tapenya lero lino kuti Mulungu anena ndi munthu, ndipo akhala ndi moyo.

25 Ndipo tsopano tiferenji? popeza mote waukuru uwu udzatitha. Tikaonjeza kumva mau a Yehova Mulungu wathu, tidzafa.

26 Pakuti ndaniyo, wa zamoyo zonse adamva mau a Mulungu wamoyo wakunena ali pakati pa moto, monga ife, nakhala ndi moyo?

27 Yandikizani inu, ndi kumva zonse Yehova Mulungu wathu adzati; ndipo inu munene ndi ife zonse zimene Yehova Mulungu wathu adzanena ndi inu; ndipo ife tidzazimva ndi kuzicita.

28 Ndipo Yehova anamva mau a kunena kwanu, pamene munanena ndi ine; ndipo Yehova anati kwa ine, Ndidamva mau a kunena kwao kwa anthu awa, amene ananena ndi iwe; cokoma cokha cokha adanenaci.

29 Ha! mwenzi akadakhala nao mtima wotere wakundiopa Ine, ndi kusunga malamulo anga masiku onse, kuti ciwakomere iwo ndi ana ao nthawi zonse!

30 Muka, nuti nao, Bwererani ku mahema anu.

31 Koma iwe, uime kuno ndi Ine, ndinene ndi iwe malamulo onse, ndi malemba, ndi maweruzo, amene uziwaphunzitsa, kuti awacite m'dziko limene ndiwapatsa likhale lao lao.

32 Potero muzisamalira kucita monga Yehova Mulungu wanu anakulamulirani; musamapatuka kulamanzere kapena kulamanja.

33 Muziyenda m'njira yonse imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani, kuti mukakhale ndi moyo, ndi kuti cikukomereni, ndi kuti masiku anu acuruke m'dziko limene mudzakhala nalo lanu lanu.

6

1 Ndipo awa ndi malamulo, malemba, ndi maweruzo, amene Yehova Mulungu wanu analamulira kukuphunzitsani, kuti muziwacita m'dziko limene muolokerako kulilandira;

2 kuti muope Yehova Mulungu wanu, kusunga malemba ace onse ndi malamulo ace, amene ndikuuzani inu ndi ana anu, ndi zidzukulu zanu, masiku onse a moyo wanu, ndi kuti masiku anu acuruke.

3 Potero imvani, Israyeli, musamalire kuwacita, kuti cikukomereni ndi kuti mucuruke cicurukire, monga Yehova Mulungu wa makolo anu anena ndi inu, m'dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi.

4 Imvani, Israyeli; Yehova Mulungu wathu, Yehova ndiye mmodzi;

5 ndipo muzikonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, ndi mphamvu yanu yonse.

6 Ndipo mau awa ndikuuzanilero, azikhala pamtima panu;

7 ndipo muziwaphunzitsa mwacangu kwa ana anu, ndi kuwalankhula awa pokhala pansi m'nyumba zanu, ndi poyenda inu panjira, ndi pogona inu pansi, ndi pouka inu.

8 Ndipo muziwamanga padzanja panu ngati cizindikilo, ndipo akhale ngati capamphumi pakati pa maso anu.

9 Ndipo muziwalembera pa mphuthu za nyumba zanu, ndi pa zipata zanu.

10 Ndipo kudzakhala, Yehova Mulungu wanu atakulowetsani m'dziko limene analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isake, ndi Yakobo, kuti adzakupatsani ili; midzi yaikuru ndi yokoma, imene simunaimanga;

11 ndi nyumba zodzala nazo zokoma ziri zonse, zimene simunazidzaza, ndi zitsime zosema, zimene simunazisema, minda yampesa, ndi minda yaazitona, zimene simunazioka, ndipo mutakadya ndi kukhuta;

12 pamenepo mudzicenjere mungaiwale Yehova, amene anakuturutsani m'dziko la Aigupto, m'nyumba ya akapolo,

13 Muziopa Yehova Mulungu wanu; ndi kutumikira Iyeyu; ndipo polumbira muzichula dzina lace.

14 Musamatsata milungu yina, milungu yina ya mitundu ya anthu akuzinga inu;

15 pakuti Yehova Mulungu wanu ali pakati panu, ndiye Mulungu wansanje; kuti ungapse mtima wa Yehova Mulungu wanu, ndi kukuonongani, kukucotsani pankhope pa dziko lapansi.

16 Musamayesa Yehova Mulungu wanu, monga munamyesa m'Masa.

17 Muzisunga mwacangu malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi mboni zace, ndi malemba ace, amene anakulamulirani.

18 Ndipo muzicita zolunjika ndi zokoma pamaso pa Yehova; kuti cikukomereni, ndi kuti mulowe kukalandira dziko lokomali Yehova analumbirira makolo anu,

19 kuingitsa adani anu onse pamaso panu, monga Yehova adanena.

20 Akakufunsani ana anu m'tsogolomo, ndi kuti, Mbonizo, ndi malemba, ndi maweruzo, zimene Yehova Mulungu wathu anakulamulirani, zitani?

21 Pamenepo muzinena kwa ana anu, Tinali akapolo a Farao m'Aigupto; ndipo Yehova anatiturutsa m'Aigupto ndi dzanja lamphamvu.

22 Ndipo Yehova anapatsa zizindikilo ndi zozizwa zazikuru ndi zowawa m'Aigupto, pa Farao, ndi pa nyumba yace yonse, pamaso pathu;

23 ndipo anatiturutsa komweko, kuti atilowetse, kutipatsa dzikoli analumbirira makolo athu.

24 Ndipo Yehova anatilamulira tizicita malemba awa onse, kuopa Yehova Mulungu wathu, kuti tipindule nako masiku onse, kuti atisunge amoyo, monga lero lino.

25 Ndipo kudzakhala kwa ife cilungamo, ngati tisamalira kucita malamulo awa onse pamaso pa Yehova Mulungu wathu, monga anatilamuliraife.

7

1 Pamene Yehova Mulungu wanu atakulowetsani m'dziko limene mumkako kulilandira likhale lanu lanu, ndipo atakataya amitundu ambiri pamaso panu, Ahiti, ndi Agirigazi, ndi Aamori, ndi Akanani, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi, mitundu isanu ndi iwiri yaikuru ndi yamphamvu yoposa inu;

2 nakawapereka Yehova Mulungu wanu pamaso panu, ndipo mukawakanthe; pamenepo muwaononge konse; musapangana nao pangano, kapena kuwacitira cifundo.

3 Ndipo musakwatitsane nao; musampatsemwana wace wamwamuna mwana wanu wamkazi, kapena kutenga mwana wace wamkazi akhale wa mwana wanu wamwamuna.

4 Popeza adzapatutsa mwana wanu aleke kunditsata Ine, kuti atumikire milungu yina; potero Yehova adzapsa mtima pa inu, ndipo adzakuonongani msanga.

5 Koma muzicita nao motero: mukapasule maguwa ao a nsembe, ndi kuphwanya zoimiritsa zao, ndi kulikha zifanizo zao, ndi kutentha mafano ao osema ndi moto.

6 Pakuti inu ndinu mtundu wa anthu wopatulika wa Yehova Mulungu wanu; Yehova Mulungu wanu anakusankhani, mukhale mtundu wa pa wokha wa iye yekha, mwa mitundu yonse ya anthu akukhala pa nkhope ya dziko.

7 Yehova sanakondwera nanu, ndi kukusankhani cifukwa ca kucuruka kwanu koposa mitundu yonse yina ya anthu, kapena kucepera kwanu;

8 koma Yehova anakuturutsani ndi dzanja lamphamvu, ndi kukuombolani m'nyumba ya akapolo, m'dzanja la Farao mfumu ya Aigupto, cifukwa Yehova akukondani, ndi cifukwa ca kusunga lumbiro lija analumbirira makolo anu.

9 Cifukwa cace dziwani kuti Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu; ndiye Mulungu wokhulupirika, wakusunga cipangano ndi cifundo ndi iwo akumkonda ndi kusunga malamulo ace, kufikira mibadwo zikwi.

10 Ndipo awabwezera onse akudana ndi iye, pamaso pao, kuwaononga; sacedwa naye wakudana ndi iye, ambwezera pamaso pace.

11 Potero muzisunga malamulo, ndi malemba, ndi maweruzo, amene ndikuuzani lero kuwacita.

12 Ndipo kudzakhala, cifukwa ca kumvera inu maweruzo awa, ndi kuwasunga, ndi kuwacita, Yehova Mulungu wanu adzakusungirani cipangano ndi cifundo cimene analumbirira makolo anu;

13 ndipo adzakukondani, ndi kukudalitsani, ndi kukucurukitsani; adzadalitsanso zipatso za thupi lanu, ndi zipatso za nthaka yanu, tirigu wanu, ndi vinyo wanu, ndi mafuta anu, zoswana za ng'ombe zanu, ndi ana a nkhosa anu, m'dziko limene analumbirira makolo anu kuti adzakupatsani.

14 Mudzakhala odalitsika koposa mitundu yonse ya anthu; sipadzakhala mwamuna kapena wamkazi wosabala pakati pa inu, kapena pakati pa zoweta zanu.

15 Ndipo Yehova adzakucotserani nthenda zonse; sadzakuikirani nthenda zoipa ziri zonse za Aigupto muzidziwa zija; koma adzaziika pa onse akudana ndi inu.

16 Ndipo mudzatha mitundu yonse ya anthu amene Yehova Mulungu wanu adzapereka kwa inu; diso lanu lisawacitire cifundo; musamatumikira milungu yao; pakuti uku kudzakucitirani msampha.

17 Mukadzanena m'mtima mwanu, Amitundu awa andicurukira; ndikhoza bwanji kuwapitikitsa?

18 musamawaopa; mukumbukile bwino cimene Yehova Mulungu wanu anacitira Farao, ndi Aigupto wonse;

19 mayesero akuru maso anu anawapenya, ndi zizindikilo ndi zozizwa, ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka, zimene Yehova Mulungu wanu anakuturutsani nazo; Yehova Mulungu wanu adzatero nayo mitundu yonse ya anthu imene muwaopa.

20 Komanso Yehova Mulungu wanu adzatumiza mabvu pakati pao, kufikira ataonongeka otsalawo, ndi akubisala pamaso panu.

21 Musamaopa pamaso pao; popeza Yehova Mulungu wanu ali pakati pa inu, Mulungu wamkuru ndi woopsa.

22 Ndipo Yehova Mulungu wanu adzataya amitundu awa pang'ono pang'ono; simuyenera kuwaononga msanga, kuti zingakucurukireni zirombo.

23 Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka pamaso panu, nadzawapitikitsa ndi kupitikitsa kwakukuru, kufikira ataonongeka.

24 Adzaperekanso mafumu ao m'dzanja mwanu, ndipo muwafafanize maina ao pansi pa thambo; palibe munthu mmodzi adzaima pamaso panu, kufikira mutawaononga,

25 Mafano osema a milungu yao muwateothe ndi moto; musamasirira siliva ndi golidi ziri pa iwo, kapena kudzitengera izi; mungakodwe nazo; pakuti izi zinyansira Yehova Mulungu wanu.

26 Musamalowa naco conyansaci m'nyumba mwanu, kuti mungaonongeke konse pamodzi naco; muziipidwa naco konse, ndi kunyansidwa naco konse; popeza ndi cinthu coyenera kuonongeka konse.

8

1 Muzisamalira kucita malamulo onse amene ndikuuzani lero lino, kuti mukhale ndi moyo, ndi kucuruka, ndi kulowa, ndi kulandira dziko limene Yehova analumbirira makolo anu.

2 Ndipo mukumbukile njira yonse imene Yehova Mulungu wanu anakuyendetsani m'cipululu zaka izi makumi anai, kuti akucepetseni, kukuyesani, kudziwa cokhala mumtima mwanu, ngati mudzasunga malamulo ace, kapena iai.

3 Ndipo anakucepetsani, nakumvetsani odala, nakudyetsani ndi mana, amene simunawadziwa, angakhale makolo anu sanawadziwa; kuti akudziwitseni kuti munthu sakhala wamoyo ndi mkate wokha, koma munthu akhala wamoyo ndi zonse zakuturuka m'kamwa mwa Yehova.

4 Zobvala zanu sizinatha pathupi panu, phazi lanu silinatupa zaka izi makumi anai.

5 Ndipo muzindikire m'mtima mwanu, kuti monga munthu alanga mwana wace, momwemo Yehova Mulungu wanu akulangani inu.

6 Ndipo muzisunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda m'njira zace, ndi kumuopa.

7 Pakuti Yehova Mulungu wanu akulowetsani m'dziko lokoma, dziko la mitsinje yamadzi, la akasupe, ndi la maiwe akuturuka m'zigwa, ndi m'mapiri;

8 dziko la tirigu ndi barele, ndi mipesa, ndi mikuyu, ndi makangaza; dziko la azitona a mafuta, ndi uci;

9 dziko loti mudzadyamo mkate wosapereweza; simudzasowamo kanthu; dziko loti miyala yace nja citsulo, ndi m'mapiri ace mukumbe mkuwa.

10 Ndipo mudzadya ndi kukhuta, ndi kuyamika Yehova Mulungu wanu cifukwa ca dziko lokomali anakupatsani.

11 Cenjerani mungaiwale Yehova Mulungu wanu, ndi kusasunga malamulo ace, ndi maweruzo ace, ndi malemba ace, amene ndikuuzani lero lino;

12 kuti, mutadya ndi kukhuta, ndi kumanga nyumba zokoma, ndi kukhalamo;

13 ndipo zitacuruka ng'ombe zanu, ndi nkhosa zanu, zitacurukanso siliva wanu ndi golidi wanu, zitacurukanso zonse muli nazo;

14 mtima wanu ungatukumuke, nimungaiwale Yehova Mulungu wanu, amene anakuturutsani m'dziko la Aigupto, m'nyumba ya akapolo;

15 amene anakutsogolerani m'cipululu cacikuru ndi coopsaco, munali njoka zamoto, ndi zinkhanira, mouma mopanda madzi; amene anakuturutsirani madzi m'thanthwe lansangalabwi;

16 amene anakudyetsani m'cipululu ndi mana, amene makolo anu sanawadziwa; kuti akucepetseni, ndi kuti akuyeseni, kuti akucitireni cokoma potsiriza panu;

17 ndipo munganene m'mtima mwanu, Mphamvu yanga ndi mkono wanga wolimba zinandifunira cuma ici.

18 Koma mukumbukile Yehova Mulungu wanu, popeza ndi Iyeyu wakupatsani mphamvu yakuonera cuma; kuti akhazikitse cipangano cace cimene analumbirira makolo anu, monga cikhala lero lino.

19 Ndipo kudzakhala kuti mukaiwalatu Yehova Mulungu wanu, ndi kutsata milungu yina ndi kuitumikira, ndikucitirani mboni lero lino kuti mudzaonongeka ndithu.

20 Monga amitundu amene Yehova awaononga pamaso panu, momwemo mudzaonongeka; cifukwa ca kusamvera mau a Yehova Mulungu wanu.

9

1 Imvani Israyeli; mulikuoloka Yordano lero lino, kulowa ndi kulandira amitundu akuru ndi amphamvu akuposa inu, midzi yaikuru ndi ya malinga ofikira kuthambo,

2 anthu akuru ndi atalitali, ana a Aanaki, amene muwadziwa, amene munamva mbiri yao, ndi kuti, Adzaima ndani pamaso pa ana a Anaki?

3 Potero mudziwe lero lino, kuti Yehova Mulungu wanu ndiye amene aoloka pamaso panu ngati moto wonyeketsa; iye adzawaononga, iye adzawagwetsa pamaso panu; potero mudzawapitikitsa, ndi kuwaononga msanga, monga Yehova analankhula ndi inu.

4 Musamanena mumtima mwanu, atawapitikitsa pamaso panu Yehova Mulungu wanu, ndi kuti, Cifukwa ca cilungamo canga Yehova anandilowetsa kudzalandira dziko ili; pakuti Yehova awapitikitsa pamaso panu cifukwa ca zoipa za amitundu awa.

5 Simulowa kulandira dziko lao cifukwa ca cilungamo canu, kapena mtima wanu woongoka; koma Yehova Mulungu wanu awapitikitsa pamaso panu cifukwa ca zoipa za amitundu awa, ndi kuti akhazikitse mau amene Yehova analumbirira makolo anu, Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo.

6 Potero mudziwe, kuti Yehova Mulungu wanu sakupatsani dziko ili lokoma mulilandire, cifukwa ca cilungamo canu; pakuti inu ndinu mtundu wa aathu opulukira.

7 Kumbukilani, musamaiwala, kuti munakwiyitsa Yehova Mulungu wanu m'cipululu; kuyambira tsikuli munaturuka m'dziko la Aigupto, kufikira munalowa m'malo muno munapiktsana ndi Yehova.

8 M'Horebe momwe munautsa mkwiyo wa Yehova; ndipo Yehova anakwiya nanu kukuonongani.

9 Muja ndinakwera m'phiri kukalandira ma gome amiyala, ndiwo magome a cipangano cunene Yehova anapangana ndi inu, ndinakhala m'phiri masiku makumi anai usana ndi usiku; osadya mkate osamwa madzi.

10 Ndipo Yehova anapereka kwa ine magome awiri amiyala, olembedwa ndi cala ca Mulungu; ndipo panalembedwa pamenepo monga mwa mau onse amene Yehova adanena ndi inu m'phirimo, ali pakati pa moto, tsiku lakusonkhana.

11 Ndipo kunali, atatha masiku makumi anai usana ndi usiku, kuti Yehova anandipatsa magome awiriwo amiyala, ndiwo magome a cipangano,

12 Ndipo Yehova anati kwa ine, Uka, fulumira kutsika kuno popeza anthu ako unawaturutsa m'Aigupto wa anadziipsa; anapatuka msanga m'njira ndinawalamulirayi; anadzipangira fano loyenga.

13 Yehova ananenanso ndi ine, ndi kuti, Ndapenya anthu awa, taona, awa ndi anthu opulukira;

14 undileke, ndiwaononge, ndi kufafaniza dzina lao pansi pa thambo; ndipo ndidzakuyesa iwe mtundu wa anthu wamphamvu ndi waukuru woposa iwo.

15 Pamenepo ndinatembenuka ndi kutsika m'phiri, ndi phirilo linatentha ndi moto; ndi magome awiri a cipangano anali m'manja mwanga.

16 Ndipo ndinapenya, taonani, mudacimwira Yehova Mulungu wanu; mudadzipangira mwana wa ng'ombe woyenga; mudapatuka msanga m'njira imene Yehova adalamulira inu.

17 Pamenepo ndinagwira magome awiriwo, ndi kuwataya acoke m'manja anga awiri, ndi kuwaswa pamaso panu.

18 Ndipo ndinagwa pansi pamaso pa Yehova, monga poyamba paja, masiku makumi anai usana ndi usiku, osadya mkate osamwa madzi, cifukwa ca macimo anu onse mudacimwa, ndi kucita coipaco pamaso pa Yehova, kuutsa mkwiyo wace.

19 Pakuti ndinacita mantha cifukwa ca mkwiyo waukali, umene Yehova anakwiya nao pa inu kukuonongani, Koma Yehova anandimvera nthawi ijanso.

20 Ndipo Yehova aliakwiya kwambiri ndi Aroni kumuononga; koma ndinampempherera Aroni nthawi yomweyo.

21 Ndipo ndinatenga cimo lanu, mwana wa ng'ombe mudampangayo, ndi kumtentha ndi moto, ndi kumphwanya, ndi kumpera bwino kufikira atasalala ngati pfumbi; ndipo ndinataya pfumbi lace m'mtsinje wotsika m'phirimo.

22 Ku Tabera, ndi ku Masa, ndi ku Kibiroti Hatava, munautsanso mkwiyo wa Yehova.

23 Ndipo pamene Yehova anakutumizani kucokera ku Kadesi Barinea, ndi kuti, Kwerani, landirani dziko limene ndakupatsani; munapikisana nao mau a Yehova Mulungu wanu, osamkhulupirira, kapena kumvera mau ace.

24 Munakhala opikisana ndi Yehova kuyambira tsikuli ndinakudziwani.

25 Ndipo ndinagwa pansi pamaso pa Yehova masiku makumi anai usana ndi usiku ndinagwa pansiwa; popeza Yehova adati kuti adzakuonongani.

26 Ndipo ndinapemphera kwa Yehova ndi kuti, Yehova Mulungu, musaononga anthu anu ndi colowa canu, amene mudawaombola mwa ukulu wanu, amene munawaturutsa m'Aigupto ndi dzanja lamphamvu,

27 Kumbukilani atumiki anu, Abrahamu, Isake, ndi Yakobo; musapenyerera kupulukira kwa anthu awa, kapena coipa cao, kapena cimo lao;

28 kuti linganene dziko limene mudatiturutsako, Popeza Yehova sanakhoza kuwalowetsa m'dziko limene adanena nao, ndi popeza anadana nao, anawaturutsa kuti awaphe m'cipululu.

29 Koma iwo ndiwo anthu anu ndi colowa canu, amene mudaturutsa ndi mphamvu yanu yaikuru ndi dzanja lanu lotambasuka.

10

1 Masiku aja Yehova anati kwa ine, Dzisemere magome awiri amiyala onga oyamba aja, nukwere kuno kwa Ine m'phiriumu, nudzipangire likasa lamtengo.

2 Ndipo ndidzalembera pa magomewo mauwo anali pa magome oyamba aja amene unawaswa, ndipo uwaike m'likasamo.

3 Potero ndinapanga likasa la mtengo wasitimu, ndinasemanso magome awiri amiyala onga oyamba aja, ndi kukwera m'phirimo, magome awiri ali m'manja mwanga.

4 Ndipo analembera pamagome, monga mwa malembedwe oyamba, mau khumiwo, amene Yehova adanena ndi inu m'phirimo, ali pakati pa moto, tsiku la kusonkhanako; ndipo Yehova anandipatsa awa.

5 Ndipo ndinatembenuka ndi kutsika m'phiri, ndi kuika magome m'likasa ndinalipanga, ali m'menemo monga Yehova anandilamulira ine.

6 Ndipo ana a Israyeli anayenda ulendo wao kucokera ku zitsime za ana a Yaakani kufikira ku Mosera. Kumeneko anamwalira Aroni, ndi kumeneko anamuika; ndipo Eleazara mwana wace anacita nchito ya nsembe m'malo mwace.

7 Kucokerako anamka ulendo ku Gudigoda, ndi kucokera ku Gudigoda kumka ku Yotibata, dziko la mitsinje yamadzi.

8 Masiku aja Yehova anapatula pfuko la Levi, linyamule likasa la cipangano la Yehova, liimirire pamaso pa Yehova kumtumikira, ndi kudalitsa m'dzina lace kufikira lero lino.

9 Cifukwa cace Levi alibe gawo kapena colowa pamodzi ndi abale ace; Yehova mwini wace ndiye colowa cace, monga Yehova Mulungu wace ananena naye.

10 Ndipo ndinakhala m'phiri monga poyamba paja, masiku makumi anai usana ndi usiku; ndipo Yehova anandimvera ine pameneponso; Yehova sanafuna kukuonongani.

11 Ndipo Yehova anati kwa ine, Uka, tenga ulendo pamaso pa anthu; kuti alowe ndi kulandira dzikoli ndinalumbirira makolo ao kuti ndidzawapatsa.

12 Ndipo tsopano, Israyeli, Yehova Mulungu wanu afunanji nanu, koma kuti muziopa Yehova Mulungu wanu, kuyenda m'njira zace zonse, ndi kukonda, ndi kutumikira Yehova Mulungu wanundimtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,

13 kusunga malamulo a Yehova, ndi malemba ace, amene ndikuuzani lero kuti kukukomereni inu?

14 Taonani thambo, ndi kumwambamwamba, dziko lapansi, ndi zonse ziri m'mwemo ndi zace za Yehova Mulungu wanu.

15 Koma Yehova anakondwera nao makolo anu kuwakonda, nasankha mbeu zao zakuwatsata, ndiwo inu, mwa mitundu yonse ya anthu, monga kuli lero lino.

16 Potero dulani khungu la mitima yanu, ndipo musamapulukiranso.

17 Popeza Yehova Mulungu wanu ndiye Mulungu wa milungu, ndi Mbuye ya ambuye; Mulungu wamkuru, wamphamvu, ndi woopsa, wosasamalira nkhope za anthu, kapena kulandira cokometsera mlandu.

18 Aweruzira ana amasiye ndi mkazi wamasiye; ndipo akonda mlendo, ndi kumpatsa cakudya ndi cobvala.

19 M'mwemo mukondane naye mlendo; popeza munali alendo m'dziko la Aigupto.

20 Muziopa Yehova Mulungu wanu; mumtumikire Iyeyo; mummamatire iye, ndi kulumbira pa dzina lace.

21 Iye ndiye lemekezo lanu, Ive ndiye Mulungu wanu, amene anacita nanu zazikuru ndi zoopsa izi, mudaziona m'maso mwanu.

22 Makolo anu anatsikira ku Aigupto ndiwo anthu makumi asanu ndi awiri; ndipo Yehova Mulungu wanu anakusandulizani tsopano mucuruke ngati nyenyezi za kumwamba.

11

1 Cifukwa cace muzikonda Yehova Mulungu wanu, ndi kusunga cilangizo cace, ndi malemba ace, ndi maweruzo ace, ndi malamulo ace, masiku onse.

2 Ndipo dziwani lero lino; pakuti sindinena ndi ana anu osadziwa, ndi osapenya kulanga kwa Yehova Mulungu wanu, ukulu wace, dzanja lace lamphamvu, ndi mkono wace wotambasuka,

3 ndi zizindikilo zace, ndi nchito zace, adazicitira Farao mfumu ya Aigupto, ndi dziko lace lonse pakati pa Aigupto;

4 ndi cocitira iye nkhondo ya Aigupto, akavalo ao, ndi agareta ao; kuti anawamiza m'madzi a Nyanja Yofiira, muja anakutsatani m'mbuyo, ndi kuti Yehova anawaononga kufikira lero lino;

5 ndi cimene anakucitirani m'cipululu, kufikira munadza kumalo kuno;

6 ndi cimene anacitira Datani ndi Abiramu, ana a Eliabu, mwana wa Rubeni; muja nthaka inatsegula pakamwa pace, ndi kuwameza iwo, ndi mabanja ao, ndi mahema ao, ndi za moyo zonse zakuwatsata pakati pa Israyeli wonse.

7 Koma maso anu anapenya nchito yonse yaikuru ya Yehova anaicita.

8 Potero muzisunga malamulo onsewa ndikuuzani lero lino, kuti mukhale amphamvu, ndi kulowa ndi kulandira dziko, limene mumkako kulilandira;

9 ndi kuti masiku anu acuruke m'dziko limene Yehova analumbirira makolo anu, kuti adzawapatsa iwo ndi mbeu zao, dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi.

10 Pakuti dziko limene mumkako kulilandira ndi losanga dziko la Aigupto lija mudaturukako, kumene kuja munafesa mbeu zanu, ndi kuzithirira ndi phazi lanu, monga munda watherere;

11 koma dziko limene mumkako kulilandira ndilo dziko la mapiri ndi zigwa; limamwa madzi a mvula ya kumwamba;

12 ndilo dziko loti Yehova Mulungu wanu alisamalira, maso a Yehova Mulungu wanu akhalapo cikhalire, kuyambira caka mpaka kutsiriza caka.

13 Ndipo kudzakhala mukasamalira cisamalire malamulo anga amene ndikuuzani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu, ndi kumtumikira ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse,

14 ndidzapatsa mvula ya dziko lanu m'nyengo yace, ya myundo ndi ya masika, kuti mutute tirigu wanu, ndi vinyo wanu, ndi mafuta anu.

15 Ndipo ndidzapatsa msipu wa zoweta zanu podyetsa panu; mudzadyanso nimudzakhuta.

16 Dzicenjerani nokha, angacete mitima yanu, nimungapatuke, ndi kutumikira milungu yina, ndi kuipembedza;

17 ndi kuti Mulungu angapse mtima pa inu, a nangatseke kumwamba, kuti isowe mvula, ndi kuti nthaka isapereke zipatso zace; ndi kuti mungaonongeke msanga m'dziko lokomali Yehova akupatsani.

18 Cifukwa cace muzisunga mau anga awa mumtima mwanu ndi m'moyo mwanu; ndi kuwamanga ngati cizindikilo pamanja panu; ndipo zikhale zapamphumi pakati pa maso anu.

19 Ndipo muziwaphunzitsa ana anu, ndi kuwalankhula awa pokhala inu pansi m'nyumba mwanu, ndi poyenda inu panjira, ndi pogona inu pansi, ndi pakuuka inu pomwe.

20 Ndipo muziwalembera pa mphuthu za nyumba zanu, ndi pa zipata zanu;

21 kuti masiku anu ndi masiku a ana anu acuruke m'dziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzawapatsali, monga masiku a thambo liri pamwamba pa dziko.

22 Pakuti mukasunga cisungire malamulo awa onse amene ndikuuzani kuwacita; kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda m'njira zace zonse, ndi kummamatira;

23 Yehova adzapitikitsa amitundu awa onse pamaso panu, ndipo mudzalanda amitundu akuru ndi amphamvu oposa inu.

24 Pamalo ponse padzapondapo phazi lanu ndi panu, kuyambira cipululu ndi Lebano, kuyambira nyanjayo, nyanja ya Pirate, kufikira nyanja ya m'tsogolo, ndiwo malice anu.

25 Palibe munthu adzaima paraaso panu; Yehova Mulungu wanu adzanjenjemeretsa ndi kuopsa dziko lonse mudzapondapo, cifukwa ca inu, monga ananena ndi inu.

26 Taonani, ndirikuika pamaso panu lero dalitso ndi temberero;

27 dalitso, ngati mudzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikuuzani lero lino;

28 koma temberero, ngati simudzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi kupatuka m'njira ndikuuzani lero lino, kutsata milungu yina imene simunaidziwa.

29 Ndipo kudzakhala, atakulowetsani Yehova Mulungu wanu m'dziko limene mumkako kulilandira, munene mdalitso pa phiri la Gerizimu, ndi temberero pa phiri la Ebala.

30 Sakhala kodi tsidya lija la Yordano, m'tseri mwace mwa njira yace yolowa dzuwa, m'dziko la Akanani, akukhala m'cidikha, pandunji pace pa Giligala, pafupi pa mathunda a More?

31 Pakuti mulinkuoloka Yordano kulowa ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani; ndipo mudzacilandira colowa canu, ndi kukhalamo.

32 Potero samalirani kucita malemba ndi maweruzo onse ndiwaika pamaso panu lero lino.

12

1 Awa ndi malemba ndi maweruzo, muziwasamalirawa kuwacita m'dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu anakupatsani likhale lanu lanu, masiku onse akukhala ndi moyo inu pa dziko lapansi.

2 Muononge konse malo onse, amitundu amene mudzawalanda anatumikirako milungu yao, pa mapiri atali, ndi pa zitunda, ndi pansi pa mitengo yonse yabiriwiri;

3 nimugumule maguwa ao a nsembe, ndi kuphwanya zoimiritsa zao, ndi kutentha zifanizo zao, ndi kulikha mafano osema a milungu yao; ndipo muononge dzina lao licoke m'malomo.

4 Musamatero ndi Yehova Mulungu wanu.

5 Koma ku malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha mwa mapfuko anu onse kuikapo dzina lace, ndiko ku cokhalamo cace, muzifunako, ndi kufikako;

6 ndi kubwera nazo kumeneko nsembe zanu zopsereza, ndi nsembe zanu zophera, ndi magawo anu onse a magawo khumi, ndi nsembe yokweza ya dzanja lanu, ndi zowinda zanu, ndi nsembe zanu zaufulu, ndi zoyamba kubadwa za ng'ombe zanu, ndi za nkhosa ndi mbuzi zanu;

7 ndipo kumeneko muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, ndi kukondwera nazo zonse mudazigwira ndi dzanja lanu, inu ndi a pa banja lanu, m'mene Yehova Mulungu wanu anakudalitsani.

8 Musamadzacita monga mwa zonse tizicita kuno lero, yense kucita ciri conse ciyenera m'maso mwace;

9 pakuti mpaka lero simunafikira mpumulo ndi colowa, zimene Yehova Mulungu wanu adzakupatsani.

10 Koma mudzaoloka Yordano, ndi kukhala m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akulandiritsani; ndipo adzakupumulitsani akulekeni adani anu onse pozungulirapo, ndipo mudzakhala mokhazikika.

11 Pamenepo padzakhala malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsako dzina lace, kumeneko muzibwera nazo zonse ndikuuzanizi; nsembe zanu zopsereza, ndi nsembe zanu zophera, magawo anu onse a magawo khumi, ndi nsembe yokweza dzanja lanu, ndi zowinda zanu zosankhika zimene muzilonjezera Yehova.

12 Ndipo mudzakondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi ana anu amuna, ndi ana anu akazi, ndi anchito anu amuna, ndi anchito anu akazi, ndi Mlevi ali m'midzi mwanu, popeza alibe gawo kapena colowa pamodzi ndi inu.

13 Dzicenjerani nokha, musamapereka nsembe zanu zopsereza pamalo ponse upaona:

14 koma pamalo pamene Yehova adzasankha, mwa limodzi la mapfuko anu, pamenepo muzipereka nsembe zanu zopsereza, ndi pamenepo muzicita zonse ndikuuzani.

15 Koma monga mwa cikhumbu conse ca moyo wanu muiphe ndi kudya nyama m'midzi yanu yonse, monga mwa mdalitso wa Yehova Mulungu wanu anakupatsani; odetsa ndi oyera adyeko, monga yamphoyo ndi yangondo.

16 Mwazi wao wokha musamadya; muziuthira panthaka ngati madzi.

17 Simukhoza kudya m'mudzi mwanu limodzi la magawo khumi la tirigu wanu, kapena la vinyo wanu, kapena la mafuta anu, kapena oyambakubadwa a ng'ombe zanu kapena la nkhosa ndi mbuzi zanu, kapena zowinda zanu ziri zonse muzilonieza kapena nsembe zanu zaufulu, kapena nsembe yokweza ya m'dzanja lanu;

18 koma muzizidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu m'malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha, inu, ndi ana anu amuna, ndi ana anu akazi, ndi anchito anu amuna, ndi anchito anu akazi, ndi Mlevi ali m'mudzi mwanu; nimukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu m'zonse mudazigwira ndi dzanja lanu.

19 Dzicenjerani nokha, musataye Mlevi masiku onse akukhala inu m'dziko mwanu.

20 Akadzakuza malire a dziko lanu Yehova Mulungu wanu, monga ananena ndi inu, ndipo mukadzati, Ndidye nyama, popeza moyo wanga ukhumba kudya nyama; mudye nyama monga umo monse ukhumba moyo wanu.

21 Malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha kuikako dzina lace akakutanimphirani, muziphako ng'ombe zanu ndi nkhosa ndi mbuzi zanu zimene Yehova anakupatsani, monga ndinakuuzani, ndi kuzidya m'mudzi mwanu, monga umo monse ukhumba moyo wanu.

22 Koma monga umo amadya mphoyo ndi ngondo momwemo uzizidya; odetsa ndi oyera adyeko cimodzimodzi.

23 Koma mulimbikepo ndi kusadya mwaziwo; popeza mwazi ndiwo moyo, nimusamadya moyo pamodzi ndi nyama yace.

24 Musamadya uwu; muuthire pansi ngati madzi.

25 Musamadya uwu; kuti cikukomereni inu, ndi ana anu akudza m'mbuyo mwanu, pakucita inu zoyenera pamaso pa Yehova.

26 Zopatulika zanu zokha zimene muli nazo, ndi zowinda zanu, muzitenge, ndi kupita nazo ku malo amene Yehova adzasanka;

27 ndipo mupereke nsembe zanu zopsereza, nyama zao ndi mwazi wao, pa guwa la nsembe la Yehova Mulungu wanu; ndipo athire mwazi wa nsembe zanu zophera pa guwa la nsembe la Yehova Mulungu wanu, koma nyama yace muidye.

28 Samalirani ndi kumvera mau awa onse ndikuuzaniwa, kuti cikukomereni inu, ndi ana anu akudza m'mbuyo mwanu nthawi zonse, pocita inu zokoma ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.

29 Pamene Yehova Mulungu wanu akadzadulatu amitundu pamaso panu, kumene mulowako kuwalandira, ndipo mutawalandira, ndi kukhala m'dziko lao,

30 dzicenjerani nokha mungakodwe ndi kuwatsata, ataonongeka pamaso panu; ndi kuti mungafunsire milungu yao, ndi kuti, Amitundu awa atumikira milungu yao bwanji? ndicite momwemo inenso.

31 Musamatero ndi Yehova Mulungu wanu; pakuti ziri zonse zinyansira Yehova, zimene azida iye, iwowa anazicitira milungu yao; pakuti angakhale ana ao amuna ndi ana ao akazi awatentha m'moto, nsembe ya milungu yao.

32 Ciri conse ndikuuzani, mucisamalire kucicita; musamaoniezako, kapena kucepsako.

13

1 Akauka pakati pa inu mneneri, kapena wakulota maloto, nakakupatsani cizindikilo kapena cozizwa;

2 ndipo cizindikilo kapena cozizwa adanenaci cifika, ndi kuti, Titsate milungu yina, imene simunaidziwa, ndi kuitumikira;

3 musamamvera mau a mneneri uyu, kapena wolota maloto uyu; popeza Yehova Mulungu wanu akuyesani, kuti adziwe ngati mukonda Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse.

4 Muziyenda kutsata Yehova Mulungu wanu, ndi kumuopa, ndi kusunga malamulo ace, ndi kumvera mau ace, ndi kumtumikira iye, ndi kummamatira.

5 Ndipo mneneriyo, kapena wolota malotoyo, mumuphe; popeza ananena cosiyanitsa ndi Yehova Mulungu wanu, amene anakuturutsani m'dziko la Aigupto, nakuombolani m'nyumba ya akapolo; kuti akuceteni mutaye njira imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani muziyendamo. Potero muzicotsa coipaco pakati pa inu.

6 Mbale wanu, ndiye mwana wa mai wanu, kapena mwana wanu wamwamuna, kapena mwana wanu wamkazi, kapena mkazi wa kumtima kwanu, kapena bwenzi lanu, ndiye ngati moyo wanu wanu, akakukakamizani m'tseri, ndi kuti, Tipite titumikire milungu yina, imene simunaidziwa, inu, kapena makolo anu;

7 ndiyo milungu ya mitundu ya anthu akuzungulira inu, akukhala pafupi pali inu, kapena akukhala patali pali inu, kuyambira malekezero a dziko lapansi kufikira malekezero ena a dziko lapansi;

8 musamabvomerezana naye, kapena kumvera iye; diso lanu lisamcitire cifundo, kapena kumleka, kapena kumbisa;

9 koma muzimupha ndithu; liyambe dzanja lanu kukhala pa iye kumupha, ndi pamenepo dzanja la anthu onse.

10 Nimuzimponya miyala, kuti afe; popeza anayesa kukucetani muleke Yehova Mulungu wanu, amene anakuturutsani m'dziko la Aigupto, m'nyumba va akapolo.

11 Kuti Israyeli wonse amve, ndi kuopa, ndi kusaonieza kucita coipa cotere conga ici pakati pa inu.

12 Ukamva za umodzi wa midzi yanu, imene Yehova Mulungu wanu akupatsani kukhalako, ndi kuti,

13 Amuna ena opanda pace anaturuka pakati pa inu, naceta okhala m'mudzi mwao, ndi kuti, Timuke titumikire milungu yina, imene simunaidziwa;

14 pamenepo muzifunsira, ndi kulondola, ndi kufunsitsa; ndipo taonani, cikakhala coona, catsimikizika cinthuci, kuti conyansa cotere cacitika pakati pa inu;

15 muzikanthatu okhala m'mudzi muja ndi lupanga lakuthwa; ndi kuuononga konse, ndi zonse ziri m'mwemo, ng'ombe zace zomwe, ndi lupanga lakuthwa.

16 Ndipo muzikundika zofunkha zace zonse pakati pakhwalala pace, nimutenthe ndi moto mudzi, ndi zofunkha zace zonse konse, pamaso pa Yehova Mulungu wanu; ndipo udzakhala mulu ku nthawi zonse; asaumangenso.

17 Ndipo pasamamatire padzanja panu kanthu ka cinthu coti cionongeke; kuti Yehova a aleke mkwiyo wacewaukali, nakucitireni cifundo, ndi kukumverani nsoni, ndi kukucurukitsani monga analumbirira makolo anu;

18 pakumvera inu mau a Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ace onse amene ndikuuzani lero lino, kucita zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.

14

1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu; musamadziceka, kapena kumeta tsitsi pakati pa maso cifukwa ca akufa.

2 Popeza ndinu mtundu wa anthu opatulikira Yehova Mulungu wanu, ndipo Yehova anakusankhani mukhale mtundu wa anthu wa pa wokha wa iye yekha, mwa mitundu yonse ya anthu okhala pankhope pa dziko lapansi.

3 Musamadya conyansa ciri conse,

4 Nyamazi muyenera kumadya ndi izi: ng'ombe, nkhosa, ndi mbuzi,

5 ngondo, ndi nswala ndi mphoyo, ndi mphalapala, ndi ngoma, ndi nyumbu, ndi mbalale.

6 Ndipo nyama iri yonse yogawanika ciboda, nikhala yogawanikadi ciboda, nibzikula, imeneyo muyenera kudya.

7 Koma izi zokha simuyenera kuzidya mwa zobzikulazo, kapena zogawanika ciboda: ngamila, ndi ka'ulu, ndi mbira, popezazibzikula, komazosagawanika ciboda, muziyese zodetsa;

8 ndi nkhumba, popeza igawanika ciboda koma yosabzikula, muiyese yodetsa; musamadya nyama yao, musamakhudza mitembo yao.

9 Mwa zonse ziri m'madzi muyenera kumadya izi: ziri zonse ziri nazo zipsepse ndi mamba, zimenezi muyenera kumadya;

10 koma ziri zonse zopanda zipsepse kapena mamba musamadya; muziyese zonyansa.

11 Mbalame zosadetsazonse muyenera kumadya.

12 Koma izi ndi zimene simuyenera kumadya: mphungu, ndi nkhwazi, ndi cikambi,

13 ndi kamtema, ndi mphamba, ndi muimba monga mwa mtundu wace;

14 ndi khungubwe ali yense monga mwa mtundu wace;

15 ndi nthiwatiwa, ndi cipudo, ndi kakoa, ndi kabawi monga mwa mtundu wace;

16 ndi nkhutukutu, ndi mancici, ndi tsekwe;

17 ndi bvuwo, ndi dembu, ndi nswankhono;

18 ndi iodwa, ndi cimeza, monga mwa mtundu wace, ndi sadzu, ndi mleme.

19 Ndipo zokwawa zonse zakuuluka muziyesa zonyansa; musamazidya.

20 Mbalame zonse zosadetsa muyenera kumadya.

21 Musamadya cinthu ciri conse citafa cokha; muzipereka ico kwa mlendo ali m'mudzi mwanu, acidye ndiye; kapena ucigulitse kwa mlendo; popeza ndinu mtundu wa anthu wopatulika wa Yehova Mulungu wanu. Musamaphika mwana wa mbuzi mu mkaka wa mace.

22 Muzipereka ndithu limodzi la magawo khumi la zipatso zonse za mbeu zanu, zofuma kumunda, caka ndi caka.

23 Ndipo muzidye pamaso pa Yehova Mulungu wanu, m'malo m'mene asankhamo iye, kukhalitsamo dzina lace; limodzi la magawo khumi la tirigu wanu, la vinyo wanu, ndi la mafuta anu, ndi oyamba kubadwa a ng'ombe zanu ndi a nkhosa ndi mbuzi zanu; kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.

24 Ndipo ikakutalikirani njira kotero kuti simukhoza kulinyamula, popeza malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha, kuikapo dzina lace, akutanimphirani; atakudalitsani Yehova Mulungu wanu;

25 pamenepo mulisinthe ndarama, ndi kumanga ndarama ikhale m'dzanja mwanu, ndi kupita ku malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha;

26 ndipo mugule ndi ndaramazo ciri conse moyo wanu ukhumba, ng'ombe kapena nkhosa, kapena vinyo, kapena cakumwa colimba, kapena ciri conse moyo wanu ukufunsani; nimudye pomwepo pamaso pa Yehova Mulungu wanu, ndi kukondwera, inu ndi a pabanja panu.

27 Koma Mlevi wokhala m'mudzi mwanu, musamamtaya, popeza alibe gawo kapena colowa pamodzi ndi inu.

28 Pakutha pace pa zaka zitatu muziturutsa magawo onse a magawo khumi a zipatso zanu za caka ico, ndi kuwalinditsa m'mudzi mwanu;

29 ndipo abwere Mlevi, popeza alibe gawo kapena colowa pamodzi ndi inu, ndi mlendo, ndi ana amasiye, ndi mkazi wamasiye, okhala m'mudzi mwanu, nadye nakhute; kuti Yehova Mulungu wanu akakudalitseni mu nchito zonse za dzanja lanu muzicitazi.

15

1 Pakutha Pace pa zaka zisanu ndi ziwiri pakhale cilekerero.

2 Cilekereroco ndici: okongoletsa onse alekerere cokongoletsa mnansi wace; asacifunse kwa mnansi wace, kapena mbale wace; popeza analalikira cilekerero ca Yehova.

3 Muyenera kucifunsa kwa mlendo; koma canu ciri conse ciri ndi mbale wanu, dzanja lanu licilekerere;

4 ndiko kuti pasakhale waumphawi mwa inu; pakuti Yehova adzakudalitsani kwambiri m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colowa canu canu;

5 cokhaci mumvere cimverere mau a Yehova Mulungu wanu, kuti musamalire kucita malamulo awa onse amene ndikuuzani lero lino.

6 Popeza Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani, monza ananena nanu; ndipo mudzakongoletsa amitundu ambiri, osakongola nokha; nimudzacita ufumu pa amitundu ambiri, koma iwo sadzacita ufumu pa inu.

7 Akakhala ndi inu munthu waumphawi, ndiye wilia wa abale anu, m'umodzi wa midzi yanu, m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, musakhakala mtima wanu, kapena kuumitsa dzanja lanu kukaniza mbale wanu waumphawi;

8 koma muzimtansira dzanjalanundithu ndi kumkongoletsa ndithu zofikira kusowa kwace, monga umo amasowa.

9 Dzicenjerani, mungakhale mau opanda pace mumtima mwanu, ndi kuti, Cayandika caka cacisanu ndi ciwiri, caka ca cilekerero; ndipo diso lanu lingaipire mbale wanu waumphawi, osampatsa kanthu; ndipo iye angalirire inu kwa Yehova; ndipo mwa inu mungakhale cimo.

10 Muzimpatsa ndithu, osawawa mtima wanu pompatsa; popeza, cifukwa ca ici Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mu nchito zanu zonse, ndi m'zonse muikapo dzanja lanu.

11 Popeza waumphawi salekana m'dziko, cifukwa cace ndikuuzani ndi kuti, Dzanja lanu mulitansire ndithu mbale wanu, ndi ozunzika anu, ndi aumphawi anu, a m'dziko mwanu.

12 Mukagula mbale wanu, Mhebri wamwamuna kapena Mhebri wamkazi, ndipo adzakutumikira zaka zisanu ndi cimodzi; koma caka cacisanu ndi ciwiri umlole acoke kwanu waufulu.

13 Ndipo pomlola iwe acoke kwanu waufulu, musamamlola acoke wopanda kanthu;

14 mumlemeze nazo za nkhosa ndi mbuzi zanu, ndi za padwale, ndi za mosungira vinyo; monga Yehova Mulungu wanu anakudalitsani mumninkhe uyu.

15 Ndipo mukumbukile kuti munali akapolo m'dziko la Aigupto, ndipo Yehova Mulungu wanu anakuombolani; cifukwa cace ndikuuzani ici lero lino.

16 Ndipo kudzakhala, akanena ndi inu, Sindituruka kucoka kwanu; popeza akonda inu ndi nyumba yanu, popeza kumkomera kwanu;

17 pamenepo muzitenga lisungulo, ndi kulipisa m'khutu mwace, kulikanikiza ndi citseko, ndipo adzakhala kapolo wanu kosalekeza. Muzicitanso momwemo ndi adzakazi anu.

18 Musamayesa neosautsa, pomlola akucokereni waufulu; popeza anakugwirirani nchito zaka zisanu ndi cimodzi monga wolipidwa wakulandira cowirikiza; potero Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani m'zonse muzicita.

19 Zazimuna zonse zoyamba kubadwa, zobadwa mwa ng'ombe zanu ndi mwa nkhosa ndi mbuzi zanu, muzizipatulira Yehova Mulungu wanu; musamagwiritsa nchito yoyamba kubadwa mwa ng'ombe zanu, kapena kusenga yoyamba kubadwa ya nkhosa kapena mbuzi zanu.

20 Muzidye caka ndi caka pamaso pa Yehova Mulungu wanu, m'malo amene Yehova adzasankha, inu ndi a m'banja mwanu.

21 Koma ikakhala naco cirema, yotsimphina, kapena yakhungu, cirema ciri conse coipa, musamaiphera nsembe Yehova Mulungu wanu.

22 Muidye m'mudzi mwanu; odetsa ndi oyera aidye cimodzimodzi, monga mphoyo ndi nswala.

23 Mwazi wace wokha musamadya; muuthire pansi ngati madzi.

16

1 Samalirani mwezi wa Abibu, kuti muzicitira Yehova Mulungu wanu Paskha; popeza m'mwezi wa Abibu Yehova Mulungu wanu anakuturutsani m'dziko la Aigupto usiku.

2 Ndipo muziphera Yehova Mulungu wanu nsembe ya Paskha, ya nkhosa ndi ya ng'ombe, m'malo amene Yehova adzasankha kukhalitsamo dzina lace.

3 Musamadyera nayo mkaye wa cotupitsa; masiku asanu ndi awiri mudyere nayo mkate wopanda cotupitsa, ndiwo mkate wa cizunziko popeza munaturuka m'dziko la Aigupto mofulumira; kuti inu kumbukile tsiku loturuka inu m'dziko la Aigupto masiku onse a moyo wanu.

4 Ndipo m'malire mwanu monse musaoneke cotupitsa masiku asanu ndi awiri; nyama yomwe muiphere nsembe tsiku loyamba madzulo, isatsaleko usiku wonse kufikira m'mawa.

5 Simuyenera kuphera nsembe ya Paskha m'midzi yanu iri yonse, imene Yehova Mulungu wanu akupatsani;

6 koma pamalo pamene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsapo dzina lace, pamenepo muphere nsembe ya Paskha, madzulo, polowa dzuwa, nyengo ya kuturuka inu m'Aigupto.

7 Ndipo muiphike ndi kuidya m'malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha; koma m'mawa mwace mubwerere kumka ku mahema anu.

8 Masiku asanu ndi limodzi muzidya mkate wopanda cotupitsa; ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri ndilo loletsa, la Yehova Mulungu wanu; musamagwira nchito pamenepo.

9 Mudziwerengere masabata asanu ndi awiri; muyambe kuwerenga masabata asanu ndi awiri poyambira kuceka tirigu waciriri.

10 Ndipo mucitire Yehova Mulungu wanu madyerero a masabata, ndiwo msonkho waufulu wa dzanja lanu, umene mupereke monga Yehova Mulungu wanu akudalitsani.

11 Ndipo mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi ana anu amuna, ndi ana anu akazi, ndi anchito anu amuna, ndi anchito anu akazi, ndi Mlevi wokhala m'mudzi mwanu, ndi mlendo, ndi mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye, okhala pakati pa inu, m'malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsako dzina lace.

12 Ndipo mukumbukire kuti munali akapolo m'Aigupto; musamalire kucita malemba awa.

13 Mudzicitire madyerero a misasa masiku asanu ndi awiri, mutasunga za padwale ndi za mopondera mphesa;

14 nimukondwere m'madyerero mwanu, inu, ndi ana anu amuna, ndi ana anu akazi, ndi anchito anu amuna, ndi anchito anu akazi, ndi Mlevi, ndi mlendo, ndi mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye okhala m'mudzi mwanu.

15 Masiku asanu ndi awiri mucitire Yehova Mulungu wanu madyerero m'malo amene Yehova adzasankha; popeza Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani m'zipatso zanu zonse, ndi m'nchito zonse za manja anu; nimukondwere monsemo.

16 Amuna onse azioneka pamaso pa Yehova Mulungu wanu m'malo amene iye adzasankha, katatu m'caka; pa madyerero a mkate wopanda cotupitsa, pa madyerero a masabata, ndi pa madyerero a misasa; ndipo asaoneke pamaso pa Yehova opanda kanthu;

17 apereke yense monga mwa mphatso ya m'dzanja lace, monga mwa mdalitso wa Yehova Mulungu wanu anakupatsani.

18 Mudziikire oweruza ndi akapitao m'inidzi yanu yonse imene Yehova Mulungu wanu akupatsani, monga mwa mapfuko anu; ndipo aweruze anthu ndi ciweruzo colungama.

19 Musamapotoza ciweruzo, musamasamalira munthu, kapena kulandira cokometsera mlandu; popeza cokometsera mlandu cidetsa maso a anzeru, niciipsa mau a olungama.

20 Cilungamo, cilungamo ndico muzicitsata, kuti mukhale ndi moyo ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani.

21 Musamadziokera mitengo iri yonse ikhale nkhalango pafupi pa guwa la nsembe la Yehova Mulungu wanu, limene mwadzimangira.

22 Ndipo musamadziutsira coimiritsa ciri conse cimene Yehova Mulungu wanu adana naco.

17

1 Musamaphera Yehova Mulungu wanu nsembe ya ng'ombe, kapena nkhosa, yokhala naco cirema, kapena ciri conse coipa; pakuti cinyansira Yehova Mulungu wanu.

2 Akapeza pakati panu, m'mudzi wanu wina umene anakupatsani Yehova Mulungu wanu, wamwamuna kapena wamkazi wakucita ciri coipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu, ndi kulakwira cipangano cace,

3 nakatumikira milungu yina, naigwadira iyo, kapena dzuwa, kapena mwezi, kapena wina wa khamu la kuthambo, losauza Ine;

4 ndipo akakuuzani, nimudamva, pamenepo muzifunsitsa, ndipo taonani, cikakhala coonadi, coti nzenizeni, conyansaci cacitika m'Israyeli;

5 pamenepo muturutse mwamunayo kapena mkaziyo, anacita coipaco, kumka naye ku zipata zanu, ndiye wamwamuna kapena wamkazi; ndipo muwaponye miyala, kuti afe.

6 Pakamwa pa mboni ziwiri kapena zitatu amuphe iye amene akuti afe; asamuphe pakamwa pa mboni imodzi.

7 Liyambe kumgwera dzanja la mboniyo kumupha; pamenepo dzanja la anthu onse, Potero muzicotsa coipaco pakati panu.

8 Ukakulakani mlandu pouweruza, ndiwo wakunena zamwazi, kapena zakutsutsana, kapena zakupandana, ndiyo mirandu yakutengana m'midzi mwanu; pamenepo muziuka ndi kukwera kumka ku malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha;

9 nimufike kwa ansembe, Alevi, ndi kwa woweruza wa m'masiku awo; nimufunsire; ndipo adzakufotokozerani maweruzidwe ace.

10 Ndipo mucite monga momwe ananena mau akufotokozeraniwo, ku malo amene Yehova adzawasankha; nimusamalire kucita monga mwa zonse akulangizanizi,

11 Monga momwe anena malamulo akulangizani, ndi monga mwa ciweruzo akufotokozerani, mucite; mau akufotokozerani musawapatukire kulamanja kapena kulamanzere.

12 Koma munthu wakucita modzikuza, osamvera wansembe wokhala ciriri kutumikirako pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kapena woweruza, munthuyo afe; ndipo mucotse coipaco kwa Israyeli.

13 Ndipo anthu onse adzamva ndi kucita mantha, osacitanso modzikuza.

14 Mutakalowa m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, ndi kulilandira lanu lanu, ndi kukhalamo; ndipo mukanena, Tidziikire mfumu, monga amitundu onse akutizinga;

15 mumuiketu mfumu yanu imene Yehova Mulungu wanu adzaisankha; wina pakati pa abale anu mumuike mfumu yanu; simuyenera kudziikira mlendo, wosakhala mbale wanu.

16 Koma asadzicurukitsire akavalo iye, kapena kubwereretsa anthu amke ku Aigupto, kuti acurukitse akavalo; popeza Yehova anati nanu, Musamabwereranso njira iyi.

17 Ndipo asadzicurukitsire akazi, kuti ungapatuke mtinta wace; kapena asadzicurukitsire kwambiri siliva ndi golidi.

18 Ndipo kudzali, pakukhala iye pa mpando wacifumu wa ufumu wace, adzilemberere cofanana ca cilamuloici m'buku, acitenge pa ici ciri pamaso pa ansembe Alevi;

19 ndipo azikhala naco, nawerengemo masiku onse a moyo wace; kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wace, kusunga mau ons acilamulo ici ndi malemba awa, kuwacita;

20 kuti mtima wace usadzikuze pa abaleace, ndi kuti asapatukire lamulolo, kulamanja kapena kulamanzere; kuti acuruke masiku ace, m'ufumu wace, iye ndi ana ace pakati pa Israyeli.

18

1 Ansembe Alevi, pfuko lonse la Levi, alibe gawo kapena colowa pamodzi ndi Israyeli; azizidya nsembe zamoto za Yehova, ndi colowa cace,

2 Alibe colowa pakati pa abale ao; Yehova mwini wace ndiye colowa cao, monga ananena nao.

3 Ndipo zoyenera ansembe, awapatse anthu akuphera nsembe ndizo: ingakhale ng'ombe kapena nkhosa azipatsa wansembe mwendo wamwamba, ndi ya m'masaya ndi chipfu.

4 Zipatso zoyamba za tirigu wanu, za vinyo wanu, ndi za mafuta anu ndi ubweya woyamba kuusenga, muwapatse izi.

5 Popeza Yehova Mulungu wanu anawasankha mwa mapfuko anu onse, aimirire natumikire m'dzina la Yehova, iwo ndi ana ao amuna kosalekeza.

6 Ndipo Mlevi akacokera ku mudzi wanu wina m'Israyeli monse, kumene akhalako, nakadza ndi cifuniro conse ca moyo wace ku malo amene Yehova adzasankha;

7 pamenepo azitumikira m'dzina la Yehova Mulungu wace, monga amacita abale ace onse Alevi akuimirirako pamaso pa Yehova.

8 Cakudya cao cizifanana, osawerengapo zolowa zace zogulitsa.

9 Mutakalowa m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, musamaphunzira kucita mongamwa zonyansa za amitundu aja.

10 Asapezeke mwa inu munthu wakupitiriza mwana wace wamwamuna kapena mwana wace wamkazi ku mota wa ula, wosamalira mitambo, kapena wosamalira kulira kwa mbalame, kapena wanyanga.

11 Kapena wotsirika, kapena wobwebweta, kapena wopenduza, kapena wofunsira akufa.

12 Popeza ali yense wakucita izi Yehova anyansidwa naye; ndipo cifukwa ca zonyansa izi Yehova Mulungu wanu awapitikitsa pamaso panu.

13 Mukhale angwiro ndi Yehova Mulungu wanu.

14 Pakuti amitundu awa amene mudzawalandira, amamvera iwo akuyesa mitambo, ndi a ula; koma inu, Yehova Mulungu wanu sakulolani kucita cotero.

15 Yehova Mulungu wanu adzakuukitsirani mneneri wa pakati panu, wa abale anu, wonga ine; muzimvera iye;

16 monga mwa zonse munafunsa Yehova Mulungu wanu m'Horebe, tsiku lakusonkhana lija, ndi kuti, Tisamvenso mau a Yehova Mulungu wathu, ndipo tisaonenso mota waukuru uwu, kuti tingafe.

17 Ndipo Yehova anati kwa ine, Cokoma ananenaci.

18 Ndidzawaukitsira mneneri wa pakati pa abale ao, wonga iwe; ndipo ndidzampatsa mau anga m'kamwa mwace, ndipo adzanena nao zonse ndimuuzazi.

19 Ndipo kudzakhala kuti munthu wosamvera mau anga amene amanena m'dzina langa, ndidzamfunsa.

20 Koma mneneri wakucita modzikuza ndi kunena mau m'dzina langa, amene sindinamlamulira anene, kapena kunena m'dzina la milungu yina, mneneri ameneyo afe.

21 Ndipo mukati m'mtima mwanu, Tidzazindikira bwanji mau amene Yehova sananena?

22 Mneneri akanena m'dzina la Yehova, koma mau adanenawa sacitika, nisafika, ndiwo mau Yehova sanawanena; mneneriyo ananena modzikuza, musamuopa iye.

19

1 Pamene Yehova Mulungu wanu ataononga amitundu, amene Yehova Mulungu wanu akupatsani dziko lao, ndipo mutalilandira lanu lanu, ndi kukhala m'midzi mwao, ndi m'nyumba zao;

2 pamenepo mudzipatulire midzi itatu pakati pa dziko lanu, limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanu lanu.

3 Mudzikonzere njira, ndi kugawa malire a dziko lanu, limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanu lanu, patatu; kuti wakupha munthu athawireko.

4 Ndipo mlandu wa munthu wakupha mnzace wakuthawirako nakhala ndi moyo ndiwo: wakupha mnzace osati dala, osamuda kale lonse;

5 monga ngati munthu analowa kunkhalango ndi mnzace kutema mitengo, ndi dzanja lace liyendetsa nkhwangwa kutema mtengo, ndi nkhwangwa iguruka m'mpinimo, nikomana ndi mnzace, nafa nayo; athawire ku wina wa midzi iyi, kuti akhale ndi moyo;

6 kuti wolipsa mwazi angalondole wakupha mnzace, pokhala mtima wace watentha, nampeza, popeza njira njaitali, namkantha kuti wafa; angakhale sanaparamula imfa, poona sanamuda kale lonse.

7 Cifukwa cace ndikuuzani ndi kuti, Mudzipatulire midzi itatu.

8 Ndipo Yehova Mulungu wanu akakulitsa malire anu, monga analumbirira makolo anu, ndi kukupatsani dziko lonse limene ananena kwa makolo anu kuwapatsa ili;

9 ukadzasunga lamulo ili lonse kulicita, limene ndikuuzani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu, ndi kuyenda m'njira zace masiku onse; pamenepo mudzionjezere midzi itatu yina pamodzi ndi itatu iyi;

10 kuti angakhetse mwazi wosacimwa pakati pa dziko lanu, limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colowa canu, pangakhale mwazi pa inu.

11 Koma munthu akamuda mnzace, namlalira, ndi kumuukira ndi kumkanth a moyo wace, kuti wafa; nakathawira ku wina wa midzi iyi;

12 pamenepo akuru a mudzi wace atumize ndi kumtengako ndi kumpereka m'manja mwa wolipsa mwazi, kuti afe.

13 Diso lanu lisamcitire cifundo, koma mucotse mwazi wosacimwa m'Israyeli, kuti cikukomereni.

14 Musamasendeza malire a mnansi wanu, amene adawaika iwo a kale lomwe, m'colowa canu mudzalandiraci, m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanu lanu.

15 Mboni imodzi isamaukira munthu pa mphulupulu iri yonse, kapena cimo liri lonse adalicimwa; pakamwa pa mboni ziwiri, kapena pakamwa pa mboni zitatu mlandu utsimikizike.

16 Mboni yaciwawa ikaukira munthu kumneneza ndi kuti analakwa;

17 pamenepo anthu onse awiri, pakati pao pali makaniwo, aziima pamaso pa Yehova, pamaso pa ansembe ndi oweruza okhala m'masiku awa;

18 ndipo oweruza afunsitse bwino; ndipo taonani, mboniyo ikakhala mboni yonama, yomnamizira mbale wace;

19 mumcitire monga iye anayesa kumcitira mbale wace; motero mucotse coipaco pakati panu.

20 Ndipo otsalawo adzamva, nadzaopa, ndi kusacitanso monga coipaco pakati panu.

21 Ndipo diso lanu lisacite cifundo, moyo kulipa moyo, diso kulipa diso, dzino kulipa dzino, dzanja kulipa dzanja, phazi kulipa phazi.

20

1 Pamene muturuka pa mdani wanu kunkhondo, ndi kuona akavalo ndi magareta ndi anthu akucurukira inu, musawaopa; popeza Yehova Mulungu wanu, amene anakukwezani kukuturutsani m'dziko la Aigupto, ali ndi inu.

2 Ndipo kudzali, pamene muyandikiza kunkhondo, ayandikize wansembe nanene ndi anthu,

3 nati nao, Tamverani, Israyeli, muyandikiza kunkhondo lero paadani anu; musalumuka mitima yanu; musacita mantha, kapena kunjenjemera, kapena kuopsedwa pamaso pao;

4 pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye wakumuka nanu, kugwirira inu pa adani anu, kukupulumutsani.

5 Ndipo akapitao anene ndi anthu, ndi kuti, Ndani munthuyo anamanga nyumba yatsopano, osalowamo? amuke nabwerere kunyumba kwace, kuti angafe kunkhondo nangalowemo munthu wina.

6 Ndipo ndani munthuyo ananka munda wamphesa osalawa zipatso zace? amuke nabwerere ku nyumba yace, kuti angafe kunkhondo, nangalawe munthu wina zipatso zace.

7 Ndipo munthuyo ndani anapala bwenzi ndi mkazi osamtenga? amuke nabwerere kunyumba kwace, kuti angafe kunkhondo, nangamtenge munthu wina.

8 Pamenepo akapitao anenenso kwa anthu, ndi kuti, Munthuyo ndani wakucita mantha ndi wofumuka mtima? amuke nabwerere kunyumba kwace, ingasungunuke mitima ya abale ace monga mtima wace.

9 Ndipo kudzali, atatha akapitao kunena ndi anthu, aike akazembe a makamu atsogolere anthu.

10 Pamene muyandikiza mudzi kucita nao nkhondo, muziupfuulira ndi mtendere.

11 Ndipo kudzali, ukakubwezerani mau a mtendere, ndi kukutsegulirani, pamenepo anthu onse opereka m'mwemo akhale alambi anu, nadzakutumikirani.

12 Koma ukapanda kucita zamtendere ndi inu, koma kucita nkhondo nanu, pamenepo uumangire tsasa.

13 Ndipo pamene Yehova Mulungu wanu aupereka m'dzanja lanu, mukanthe amuna ace onse ndi lupanga lakuthwa.

14 Koma akazi ndi ana ndi ng'ombe ndi zonse ziti m'mudzimo, zankhondo zace zonse, mudzifunkhire nokha; ndipo mudye zankhondo za adani anu, zimene Yehova Mulungu wanu anakupatsani.

15 Muzitero nayo midzi yonse yokhala kutaritari ndi inu, yosakhala midzi ya amitundu awa.

16 Koma za midzi ya amitundu awa, imene Yehova Mulungu wanu akupatsani, ikhale colowa canu, musasiyepo camoyo ciri conse cakupuma;

17 koma muwaononge konse Ahiti, ndi Aamori, Akanani, ndi Aperizi, Ahivi ndi Ayebusi; monga Yehova Mulungu wanu anakulamulirani;

18 kuti angakuphunzitseni kucita monga mwa zonyansa zao zonse, amazicitira milungu yao; ndipo mungacimwire Yehova Mulungu wanu.

19 Pamene mumangira tsasa mudzi masiku ambiri, pouthirira nkhondo kuugwira, usamaononga mitengo yace ndi kuitema ndi nkhwangwa; pakuti ukadyeko, osailikha; pakuti mtengo wa m'munda ndiwo munthu kodi kuti uumangire tsasa?

20 Koma mitengo yoidziwa inu kuti si ndiyo mitengo yazipatso, imeneyi muiononge ndi kuilikha; ndipo mudzi wocita nanu nkhondo muumangire macemba, mpaka mukaugonjetsa.

21

1 Akapeza munthu waphedwa m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanu lanu, nagona pamunda, wosadziwika wakumkantha,

2 pamenepo azituruka akuru anu ndi oweruza anu, nayese ku midzi yomzinga wophedwayo;

3 ndipo kudzali kuti mudzi wakukhala kufupi kwa munthu wophedwayo, inde akuru a mudzi uwu atenge ng'ombe yamsoti yosagwira nchito, yosakoka goli;

4 ndipo akuru a mudzi uwu atsike nao msotiwo ku cigwa coyendako madzi, cosalima ndi cosabzala, naudula khosi msotiwo m'cigwamo;

5 ndipo ansembe, ana a Levi, ayandikize; pakuti Yehova Mulungu wanu anasankha iwo kumtumikira ndi kudalitsa m'dzina la Yehova; ndipo kutengana konse ndi kupandana konse kukonzeke monga mwa mau awa.

6 Ndipo akuru onse a mudziwo wokhala pafupi pa munthu wophedwayo azisamba manja ao pa msoti woudula khosi m'cigwamo;

7 nayankhe nati, Manja athu sanakhetsa mwazi uwu, ndi maso athu sanauona.

8 Landirani, Yehova, cotetezera anthu anu Israyeli, amene munawaombola, ndipo musalole mwazi wosacimwa ukhale pakati pa anthu anu Israyeli; ndipo adzawatetezera ca mwaziwo.

9 Cotero mudzicotsere mwazi wosacimwa pakati panu, pakuti wacita coyenera pamaso pa Yehova.

10 Pamene muturuka kumka ku nkhondo ya pa adani anu, ndipo Yehova Mulungu wanu awapereka m'manja mwanu, ndipo muwagwira akhale akapolo anu;

11 mukaona mwa akapolowa mkazi wokongola, mukamkhumba, ndi kufuna kumtenga akhale mkazi wanu;

12 pamenepo mufike naye kwanu ku nyumba yanu; ndipo amete tsitsi la pamutu pace, ndi kuwenga makadabo ace;

13 nabvule zobvala za ukapolo wace, nakhale m'nyumba mwanu, nalire atate wace, ndi mai wace mwezi wamphumphu; ndipo atatero mulowe naye ndi kukhala mwamuna wace, ndi iye akhale mkazi wanu.

14 Ndipo kudzali, mukapanda kukondwera naye, mumlole apite komwe afuna; koma musamgulitsa ndalama konse, musamamuyesa cuma, popeza wamcepetsa.

15 Munthu akakhala nao akazi awiri, wina wokondana naye, wina wodana naye, nakambalira ana, wokondana naye, ndi wodana naye yemwe; ndipo mwana wamwamuna woyamba akakhala wa iye uja anadana naye;

16 pamenepo kudzali, tsiku lakugawira ana ace amuna cuma cace, sangakhoze kuyesa mwana wa wokondana naye woyamba kubadwa, wosati mwana wa wodana naye, ndiye woyamba kubadwatu.

17 Koma azibvomereza wobadwa woyamba, mwana wa wodana naye, ndi kumwirikizira gawo lace la zace zonse; popeza iye ndiye ciyambi ca mphamvu yace; zoyenera woyamba kubadwa nzace.

18 Munthu akakhala naye mwana wamwamuna wopulukira, ndi wopikisana naye, wosamvera mau a atate wace, kapena mau a mai wace, wosawamvera angakhale anamlanga;

19 azimgwira atate wace ndi mai wace, ndi kuturukira naye kwa akuru a mudzi wace, ndi ku cipata ca malo ace;

20 ndipo anene kwa akulu a mudzi wace, Mwana wathu wamwamuna uyu ngwopulukira ndi wopikisana nafe, wosamvera mau athu, ndiye womwazamwaza, ndi woledzera.

21 Pamenepo amuna onse a mudzi wace amponye miyala kuti afe; cotero mucotse coipaco pakati panu; ndipo Israyeli wonse adzamva, nadzaopa.

22 Munthu akakhala nalo cimo loyenera imfa, kuti amuphe, ndipo wampacika;

23 mtembo wace usakhale pamtengo usiku wonse, koma mumuike ndithu tsiku lomwelo; pakuti wopacikidwa pamtengo atembereredwa ndi Mulungu; kuti mungadetse dziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colowa canu.

22

1 Mukapenya ng'ombe kapena nkhosa ya mbale wako zirikusokera musamazilekerera, muzimbwezera mbale wanu ndithu.

2 Ndipo ngati mbale wanu sakhala pafupi ndi inu, kapena mukapanda kumdziwa, mubwere nayo kwanu ku nyumba yanu, kuti ikhale kwanu, kufikira mbale wanu akaifuna, ndipo wambwezera iyo.

3 Mutero nayenso buru wace; mutero naconso cobvala cace; mutero naconso cotayika ciri conse ca mbale wanu, cakumtayikira mukacipeza ndi inu; musamazilekerera.

4 Mukapenya buru kapena ng'ombe ya mbale wanu, zitagwa m'njira, musamazilekerera; mumthandize ndithu kuziutsanso.

5 Mkazi asabvale cobvala ca mwa muna, kapena mwamuna asabvale cobvala ca mkazi; pakuti ali yense wakucita izi Yehova Mulungu wanu anyansidwa naye.

6 Mukacipeza cisa ca mbalame panjira, mumtengo kapena panthaka pansi, muli ana kapena mazira, ndi mace alikuumatira ana kapena mazira, musamatenga mace pamodzi ndi ana;

7 muloletu mace amuke, koma mudzitengere ana; kuti cikukomereni, ndi kuti masiku anu acuruke.

8 Pamene mumanga nyumba yatsopano, muzimanga kampanda pa tsindwi lace, kuti ungatengere nyumba yanu mwazi, akagwako munthu.

9 Musamabzala mbeu zosiyana m'munda wanu wamphesa, kuti zingaipsidwe mbeu zonse udazibzala, ndi zipatso za munda wamphesa zomwe.

10 Musamalima ndi buru ndi ng'ombe zikoke pamodzi.

11 Musamabvala nsaru yosokonezeka yaubweya pamodzi ndi thonje.

12 Mudzipangire mphonje pa ngondya zinai za copfunda canu cimene mudzipfunda naco.

13 Munthu akatenga mkazi, nalowana naye, namuda,

14 namneneza zoutsa mbiri yamanyazi, ndi kumveketsa dzina loipa, ndi kuti, Ndinamtenga mkazi uyu, koma polowana nave sindinapeza zizindikilo zakuti ndiye namwali ndithu;

15 pamenepo atate wa namwaliyo ndi mai wace azitenga ndi kuturuka nazo zizindikilo za unamwali wace wa namwaliyo, kumka nazo kwa akuru a mudzi kucipata;

16 ndipo atate wa namwaliyo azinena kwa akuru, Ndinampatsa munthuyu mwana wanga wamkazi akhale mkazi wace, koma amuda;

17 ndipo, taonani, wamneneza zoutsa mbiri yamanyazi, ndi kuti, Sindinapeza zizindikilo za unamwali wace in'mwana wako wamkazi; koma si izi zizindikilo za unamwali wa mwana wanga wamkazi. Ndipo azifunyulula cobvalaco pamaso pa akulu a mudziwo.

18 Pamenepo akuru a mudziwo azitenga munthuyu ndi kumkwapula;

19 ndi kumlipitsa masekeli makumi okha okha khumi a siliva, ndi kuipereka kwa atate wa namwaliyo, popeza anamveketsa dzina loipa namwali wa Israyeli, ndipo azikhala mkazi wace, sakhoza kumcotsa masiku ace onse.

20 Koma cikakhala coona ici, kuti zizindikilo zakuti ndiye namwali zidamsowa namwaliyo;

21 pamenepo azimturutsa namwaliyo ku khomo la nyumba ya atate wace, ndipo amuna a mudzi wace azimponya miyala kuti afe; popeza anacita copusa m'Israyeli, kucita cigololo m'nyumba ya atate wace; cotero uzicotsa coipaco pakati panu.

22 Akampeza munthu alikugona ndi mkazi wokwatibwa ndi mwamuna; afe onse awiri, mwamuna wakugona ndi mkazi, ndi mkazi yemwe; cotero muzicotsa coipaco mwa Israyeli.

23 Pakakhala namwali, wosadziwa mwamuna, wopalidwa ubwenzi ndi mwamuna, ndipo anampeza m'mudzi mwamuna, nagona nave;

24 muziwaturutsa onse awiri kumka nao ku cipata ca mudzi uwo, ndi kuwaponya miyala kuti afe; namwaliyo popeza sanapfuula angakhale anali m'mudzi; ndi mwamuna popeza anacepetsa mkazi wa mnansi wace; cotero muzicotsa coipaco pakati panu.

25 Koma mwamuna akapeza namwali wopalidwa bwenzi kuthengo, namgwira mwamunayo, nagona naye; pamenepo afe mwamuna yekha wogona naye;

26 koma namwaliyo musamamcitira kanthu; namwaliyo alibe cimo loyenera imfa; pakuti mlandu uwu ukunga munthu waukira mnzace namupha;

27 pakuti anampeza kuthengo; namwali wopalidwa bwenziyo anapfuula, koma panalibe wompulumutsa.

28 Munthu akapeza namwali wosadziwa mwamuna, ndiye wosapalidwa ubwenzi, oakamgwira nagona naye, napezedwa iwo,

29 pamenepo mwamuna amene anagona naye azipatsa atate wace wa namwaliyo masekeli makumi asanu a siliva, ndipo azikhala mkazi wace; popeza anamcepetsa; sakhoza kumcotsa masiku ace onse.

30 Munthu asatenge mkazi wa atate wace, kapena kubvula atate wace.

23

1 Munthu wophwetekwa, wophwanyika kapena wofulika, asalowe m'msonkhano wa Yehova.

2 Mwana wa m'cigololo asalowe m'msonkhano wa Yehova, ngakhale mbadwo wace wakhumi usalowe m'msonkhano wa Yehova.

3 M-amoni kapena Mmoabu asalowe m'msonkhano wa Yehova; ngakhale mbadwo wao wakhumi usalowe m'msonkhano wa Yehova, ku nthawi zonse;

4 popeza sanakukumikani ndi mkate ndi madzi m'njira muja munaturuka m'Aigupto; popezanso anakulembererani Balamu mwana wa Beori wa ku Petori wa Mesapotamiya, kuti akutemberereni.

5 Ndipo Yehova Mulungu wanu sanafuna kumvera Balamu; koma Yehova Mulungu wanu anakusandulizirani tembererolo likhale mdalitso, popeza Yehova Mulungu wanu anakukondani.

6 Musawafunira mtendere, kapena cowakomera masiku anu onse ku nthawi zonse.

7 Musamanyansidwa naye M-edomu, popeza ndiye mbale wanu; musamanyansidwa naye M-aigupto, popeza munali alendo m'dziko lace.

8 Ana obadwa nao a mbadwo wacitatu alowe m'msonkhano wa Yehova.

9 Nkhondo yanu ikaturuka pa adani anu, mudzisunge kusacita coipa ciri conse.

10 Pakakhala munthu pakati pa inu, ndiye wosayera cifukwa cocitika usiku, azituruka kunja kwa cigono, asalowe pakati pa cigono;

11 koma kudzali pofika madzulo, asambe m'madzi; ndipo litalowa dzuwa alowe pakati pa cigono.

12 Mukhale nao malo kunja kwa cigono kumene muzimukako kuthengo;

13 nimukhale naco cokumbira mwa zida zanu; ndipo kudzali, pakukhala inu pansi kuthengo mukumbe naco, ndi kutembenuka ndi kufotsera cakuturukaco;

14 popeza Yehova Mulungu wanu ayenda pakati pa cigono canu, kukupulumutsani ndi kupereka adani anu pamaso panu; cifukwa cace cigono canu cikhale copatulika; kuti angaone kanthu kodetsa mwa inu, ndi kukupotolokerani.

15 Musamapereka kwa mbuye wace kapolo wopulumuka kwa mbuye wace kuthawira kwa inu;

16 akhale nanu, pakati panu, ku malo asankhako iye m'mudzi mwanu mwina momkonda; musamamsautsa.

17 Pasakhale mkazi wacigololo pakati pa ana akazi a Israyeli, kapena wacigololo pakati pa ana amuna a Israyeli.

18 Musamabwera nayo mphotho ya wacigololo, kapena mtengo wace wa garu kulowa nazo m'nyumba ya Yehova Mulungu wanu, cifukwa ca cowinda ciri conse; pakuti onse awiriwa Yehova Mulungu wanu anyansidwa nao.

19 Musamakongoletsa mbale wanu mopindulitsa; phindu la ndarama, phindu la cakudya, phindu la kanthu kali konse kokongoletsa.

20 Mukongoletse mlendo mopindulitsa; koma mbale wanu musamamkongoletsa mopindulitsa, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni mwa zonse muzigwira ndi dzanja lanu, m'dziko limene mulowamo kulilandira.

21 Mukawindira Yehova Mulungu wanu cowinda, musamacedwa kucicita; popeza Yehova Mulungu wanu adzakufunsani za ici ndithu ndipo mukadacimwako.

22 Koma mukapanda kulonieza cowinda, mulibe kucimwa.

23 Coturuka pa milomo yanu mucisamalire ndi kucicita; monga munaloniezera Yehova Mulungu wanu, copereka caufulu munacilonjeza pakamwa panu.

24 Mukalowa m'munda wamphesa wa mnansi wanu, mudyeko mphesa ndi kukhuta nazo monga mufuna eni koma musaika kanthu m'cotengera canu.

25 Mukalowa m'tirigu wosasenga wa mnansi wanu, mubudule ngala ndi dzanja lanu, koma musasengako ndi zenga tirigu waciriri wa mnansi wanu.

24

1 Munthu akatenga mkazi akhale wace, kudzali, ngati sapeza ufulu pamaso pace, popeza anapeza mwa iye kanthu kosayenera, amlembere kalata wa cilekanitso, ndi kumpereka uyu m'dzanja lace, ndi kumturutsa m'nyumba mwace.

2 Ndipo ataturuka m'nyumba mwace, amuke nakhale mkazi wa mwamuna wina.

3 Ndipo akamuda mwamuna waciwiriyo, nakamlemberanso kalata wa cilekanitso, ndi kumpereka uyu m'dzanja lace, nakamturutsa m'nyumba mwace; kapena akamwalira mwamuna wotsirizayo, amene anamtenga akhale mkazi wace;

4 pamenepo mwamuna woyamba anamcotsayo sangathe kumtenganso akhale mkazi wace, atadetsedwa iye; pakuti ici ndi conyansa pamaso pa Yehova; ndipo usamacimwitsa dziko, limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colandira canu.

5 Munthu akatenga mkazi watsopano, asaturuke nayo nkhondo, kapena asamcititse kanthu kali konse; akhale waufulu ku nyumba yace caka cimodzi, nakondweretse mkazi adamtengayo.

6 Munthu asalandire cikole mphero, ngakhale mwanamphero, popeza alandirapo cikole moyo wamunthu.

7 Akampeza munthu waba mbale wace wina wa ana a Israyeli, namuyesa kapolo, kapena wamgulitsa, afe wakubayo; potero muzicotsa coipaco pakati panu.

8 Cenjerani nayo nthenda yakhate, kusamaliratu, ndi kucita monga mwa zonse akuphunzitsani ansembe Alevi; monga ndinalamulira iwo, momwemo muzisamalira kucita.

9 Kumbukilani cimene Yehova Mulungu wanu anacitira Miriamu panjira, poturuka inu m'dziko la Aigupto.

10 Mukakongoletsa mnansi wanu ngongole iri yonse, musamalowa m'nyumba mwace kudzitengera cikole cace.

11 Muime pabwalo, ndi munthu amene umkongoletsayo azituruka naco cikoleco kwa inu muli pabwalo.

12 Ndipo akakhala munthu waumphawi musagone muli naco cikole cace;

13 polowa dzuwa mumbwezeretu cikoleco, kuti agone m'cobvala cace, ndi kukudalitsani; ndipo kudzakukhalirani cilungamo pamaso pa Yehova Mulungu wanu.

14 Musamasautsa wolembedwa nchito, wakukhala waumphawi ndi wosauka, wa abale anu kapena wa alendo ali m'dziko mwanu, m'midzi mwanu.

15 Pa tsiku lace muzimpatsa kulipira kwace, lisalowepo dzuwa; pakuti ndiye waumphawi, ndi mtima wace ukhumba uku; kuti angakulirireni kwa Yehova, ndipo kukukhaireni cimo.

16 Atate asaphedwere ana, ndi ana asaphedwere atate; munthu yense aphedwere cimo lace lace.

17 Musamaipsa mlandu wa mlendo, kapena wa ana amasiye; kapena kutenga cikole cobvala ca mkazi wamasiye;

18 koma muzikumbukila kuti munali akapolo m'Aigupto, ndi kuti Yehova Mulungu wanu anakuombolaniko; cifukwa cace ndikuuzani kucita cinthu ici.

19 Mutasenga dzinthuzanu m'munda mwanu, ndipo mwaiwala mtolo m'mundamo, musabwererako kuutenga; ukhale wa mlendo, wa mwana wamasiye, ndi wa mkazi wamasiye; kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni m'nchito zonse za manja anu.

20 Mutagwedeza mtengo wanu wa azitona musayesenso nthambi mutatha nazo; akhale a mlendo, a mwana wamasiye, ndi a mkazi wamasiye.

21 Mutachera m'munda wanu wamphesa, musakunkha pambuyo panu; zikhale za mlendo, za mwana wamasiye, ndi za mkazi wamasiye.

22 Ndipo muzikumbukila kuti munali: akapolo m'dziko la Aigupto; cifukwa cace ndikuuzani kucita cinthu ici.

25

1 Pakakhala ndeu pakati pa anthu, nakapita kukaweruzidwa iwowa, nakaweruza mlandu wao oweruza; azimasula wolungama, namange woipa.

2 Ndipo kudzali, wocita coipa akayenera amkwapule, woweruza amgonetse kuti amkwapule pamaso pace, amwerengere zofikira coipa cace.

3 Amkwapule kufikira makumi anai, asaonjezepo; pakuti, akaonjezapo ndi kumkwapula mikwapulo yambiri, angapeputse mbale wanu pamaso panu.

4 Musamapunamiza ng'ombe popuntha tirigu.

5 Abale akakhala pamodzi, nafa wina wa iwowa, wopanda mwana wamwamuna, mkazi wa wafayo asakwatibwe ndi mlendo wakunja; mbale wa mwamuna wace alowane naye, namtenge akhale mkazi wace, namcitire zoyenera mbale wa mwamuna wace.

6 Ndipo kudzali, kuti woyamba kubadwa amene adzambala, adzalowa dzina lace la mbale wace wafayo, kuti dzina lace lisafafanizidwe m'Israyeli.

7 Ndipo ngati mwamunayo safuna kutenga mkazi wa mbale wace, mkazi wa mbale waceyo azikwera kumka kucipata, kwa akuru, ndi kuti, Mbale wa mwamuna wanga akana kuutsira mbale wace dzina m'Israyeli; safuna kundicitira ine zoyenera mbale wa mwamuna.

8 Pamenepo akuru a mudzi wace amuitane, ndi kulankhula naye; ndipo akaimirira ndi kuti, Sindifuna kumtenga;

9 pamenepo mkazi wa mbale wace azimyandikiza pamaso pa akuru, nacotse nsapato yace ku ph zi la mwamunayo, ndi kumthira malobvu pankhope pace, ndi kumyankha ndi kuti, Atere naye mwamuna wosamanga nyumba ya mbale wace.

10 Ndipo azimucha dzina lace m'Israyeli, Nyumba ya uje anamcotsa nsapato.

11 Akalimbana wina ndi mnzace, nakayandikiza mkazi wa winayo kulanditsa mwamuna wace m'dzanja la wompandayo, nakaturutsa dzanja lace, ndi kumgwira kudzibvalo;

12 pamenepo muzidula dzanja lace; diso lanu lisamcitire cifundo.

13 Musamakhala nayo m'thumba mwanu miyala ya miyeso iwiri, waukuru ndi waung'ono.

14 Musamakhala nayo m'nyumba yanu miyeso ya efa yosiyana, waukuru ndi waung'ono.

15 Muzikhala nao mwala wa muyeso wofikira ndi woyenera; mukhale nao muyeso wa efa wofikira ndi woyenera; kuti masiku anu acuruke m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani.

16 Pakuti onse akucita zinthu izi, onse akucita cisalungamo, Yehova Mulungu wanu anyansidwa nao.

17 Kumbukilani cocitira inu Amaleki panjira, poturuka inu m'Aigupto;

18 kuti anakomana ndi inu panjira, nakantha onse ofok a akutsala m'mbuyo mwanu, pakulema ndi kutopa inu; ndipo sanaopa Mulungu,

19 Ndipo kudzali, pamene Yehova Mulungu wanu atakupumulitsirani adani anu onse ozungulira, m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colowa canu canu, kuti muzifafaniza cikumbutso ca Amaleki pansi pa thambo; musamaiwala.

26

1 Ndipo kudzali, utakalowa m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colowa canu, ndipo mwacilandira ndi kukhala m'mwemo;

2 kuti muzitengako zoyamba za zipatso zonse za nthaka, zakubwera nazo inu zocokera m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani; ndi kuziika mumtanga, ndi kupita ku malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsako dzina lace.

3 Ndipo mufike kwa wansembe wakukhala m'masiku awa, ndi kunena naye, Ndibvomereza lero lino kwa Yehova Mulungu wako, kuti ndalowa m'dziko limene Yehova analumbirira makolo athu, kuti adzatipatsa ili.

4 Ndipo wansembe alandire mtanga m'manja mwanu, ndi kuuika pa guwa la nsembe la Yehova Mulungu wanu.

5 Ndipo muyankhe ndi kuti pamaso pa Yehova Mulungu wanu, Kholo langa ndiye M-aramu wakuti atayike, natsika kumka ku Aigupto, nagoneragonera komweko ali nao anthu pang'ono, nasandukako mtundu waukuru, wamphamvu, ndi wocuruka anthu ace;

6 koma Aaigupto anaticitira coipa, natizunza, natisenza nchito yolimba.

7 Pamenepo tinapfuulira kwa Yehova, Mulungu wa makolo athu; ndipo Yehova anamva mau athu, napenya kuzunzika kwathu, ndi nchito yathu yolemetsa, ndi kupsinjika kwathu;

8 ndipo Yehova anatiturutsa m'Aigupto ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka, ndi kuopsa kwakukuru, ndi zizindikilo, ndi zodabwiza;

9 ndipo anabwera nafe kumalo kuno, natipatsa dziko ili ndilo dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi.

10 Ndipo tsopano, taonani, ndabwera nazo zoyamba za zipatso za nthaka, zimene Inu, Yehova, mwandipatsa. Ndipo muziike pamaso pa Yehova Mulungu wanu, ndi kugwadira Yehova Mulungu wanu;

11 ndipo mukondwere nazo zokoma zonse zimene Yehova Mulungu wanu akupatsani, inu ndi nyumba zanu, inu ndi Mlevi, ndi mlendo ali pakati panu.

12 Mutatha kugawa magawo khumi, zobala zanu zonse caka cacitatu, ndico caka cogawa magawo khumi, muzizipereka kwa Mlevi, kwa mlendo, kwa mwana wamasiye, ndi kwa mkazi wamasiye, kuti adye m'midzi mwanu, ndi kukhuta.

13 Ndipo munene pamaso pa Yehova Mulungu wanu, Ndacotsa zopatulika m'nyumba mwanga, ndi kuzipereka kwa Mlevi, ndi kwa mlendo, ndi kwa mwana wamasiye, ndi kwa mkazi wamasiye, monga mwa lamulo lanu lonse munandilamulira ine; sindinalakwira malamulo anu, kapena kuwaiwala.

14 Sindinadyako m'cisoni canga, kapena kucotsako podetsedwa, kapena kuperekako kwa akufa; ndamvera mau a Yehova Mulungu wanga; ndacita monga mwa zonse munandilamulira ine.

15 Penyani muli mokhalamo mwanu mopatulika, m'mwamba, ndipo dalitseni anthu anu Israyeli, ndi nthaka imene munatipatsa, monga munalumbirira makolo athu, dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi.

16 Lero lino Yehova Mulungu wanu akulamulirani kucita malemba ndi maweruzo awa; potero muzimvera ndi kuwacita ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse.

17 Mwalonjezetsa Yehova lero kuti adzakhala Mulungu wanu, ndi kuti mudzayenda m'njira zace, ndi kusunga malemba ace, ndi malamulo ace, ndi maweruzo ace, ndi kumvera mau ace.

18 Ndipo Yehova wakulonjezetsani lero kuti mudzakhala anthu ace ace a pa okha, monga ananena ndi inu, ndi kuti mudzasunga malamulo ace onse;

19 kuti akukulitseni koposa amitundu onse anawalenga, wolemekezeka, womveka dzina, ndi waulemu; ndi kuti mukhale mtundu wa anthu wopatulikira Yehova Mulungu wanu monga ananena.

27

1 Ndipo Mose ndi akuru a Israyeli anauza anthu, nati, Sungani malamulo onse ndikuuzani lero.

2 Ndipo kudzali, tsiku lakuoloka inu Yordano kulowa dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, kuti mudziutsire miyala yaikuru, ndi kuimata ndi njeresa;

3 ndipo mulemberepo mau onse a cilamulo ici, mutaoloka; kuti mulowe m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi, monga Yehova Mulungu wa makolo anu ananena ndi inu.

4 Ndipo kudzali, mutaoloka Yordano, muutse miyala iyi ndikuuzani lero, m'phiri la Ebala, ndi kuimata ndi njeresa.

5 Ndipo komweko mumangire Yehova Mulungu wanu guwa la nsembe, guwa la nsembe lamiyala; musakwezepo cipangizo cacitsulo.

6 Mumange guwa la nsembe la Yehova Mulungu wanu lamiyala yosasema; ndi kuperekapo nsembe zopsereza kwa Yehova Mulungu wanu;

7 ndi kuphera nsembe zoyamika, ndi kudyapo, ndi kukondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.

8 Ndipo mulembere pa miyalayi mau onse a cilamulo ici mopenyeka bwino.

9 Ndipo Mose, ndi ansembe Alevi ananena ndi Israyeli wonse, ndi kuti, Khalani cete, imvanitu, Israyeli; lero lino mwasanduka mtundu wa anthu wa Yehova Mulungu wanu.

10 Potero muzimvera mau a Yehova Mulungu wanu, ndi kucita malamulo ace, ndi malemba ace, amene ndikuuzani lero lino.

11 Ndipo Mose anauza anthu tsiku lomwelo, ndi kuti,

12 Aimirire awa pa phiri la Gerizimu kudalitsa anthu, mutaoloka Yordano: Simeoni ndi Levi, ndi Yuda, ndi Isakara, ndi Yosefe, ndi Benjamini.

13 Naimirire awa pa phiri la Ebala, kutemberera: Rubeni, Gadi, ndi Aseri, ndi Zebuloni, Dani, ndi Nafitali.

14 Ndipo ayankhe Alevi ndi kunena kwa amuna onse a Israyeli, ndi mau omveka.

15 Wotembereredwa munthu wakupanga fano losema kapena loyenga, lonyansidwa nalo Yehova, nchito ya manja a mmisiri, ndi kuliika m'malo a m'tseri. Ndipo anthu onse: ayankhe ndi kuti, Amen.

16 Wotembereredwa iye wakupeputsa atate wace kapena mai wace. Ndi anthu onse anene, Amen.

17 Wotembereredwa iye wakusendeza malire a mnansi wace. Ndi anthu onse anene, Amen.

18 Wotembereredwa wakusokeretsa wakhungu m'njira, Ndi anthu onse anene, Amen.

19 Wotembereredwa iye wakuipsa mlandu wa mlendo, mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye. Ndi anthu onse anene, Amen.

20 Wotembereredwa iye wakugona ndi mkazi wa atate wace; popeza wabvula atate wace. Ndi anthu onse anene, Amen.

21 Wotembereredwa iye wakugona ndi nyama iri yonse. Ndi anthu onse anene, Amen.

22 Wotembereredwa iye wakugona ndi mlongo wace, mwana wamkazi wa atate wace, kapena mwana wamkazi wa mace. Ndi anthu onae anene, Amen.

23 Wotembereredwa iye wakugona ndi mpongozi wace. Ndi anthu onse anene, Amen.

24 Wotembereredwa iye wakukantha mnansi wace m'tseri. Ndi anthu onse anene, Amen.

25 Wotembereredwa iye wakulandira camwazi cakuti akanthe munthu wosacimwa. Ndi anthu onse anene, Amen.

26 Wotembereredwa iye wosabvomereza mau a cilamulo ici kuwacita. Ndi anthu onse anene, Amen.

28

1 Ndipo kudzali, mukadzamvera mau a Yehova Mulungu wanu mwacangu, ndi kusamalira kucita malamulo ace onse amene ndikuuzani lero, kuti Yehova Mulungu wanu adzakukulitsani koposa amitundu onse a pa dziko lapansi;

2 ndipo madalitso awa onse adzakugwerani, ndi kukupezani, mukadzamvera mau a Yehova Mulungu wanu.

3 Mudzakhala odala m'mudzi, ndi odala kubwalo.

4 Zidzakhala zodala zipatso za thupi lanu, ndi zipatso za nthaka yanu, ndi zipatso za zoweta zanu, zoswana za ng'ombe zanu, ndi zoswana za nkhosa zanu.

5 Zidzakhala zodala mtanga wanu, ndi coumbiramo mkate wanu.

6 Mudzakhala odala polowa inu, mudzakhala odala poturuka inu.

7 Yehova adzakantha adani anu akukuukirani; adzakudzerani njira imodzi, koma adzathawa pamaso panu njira zisanu ndi ziwiri.

8 Yehova adzakulamulirani dalitso m'nkhokwe zanu, ndi m'zonse muturutsirako dzanja lanu; ndipo adzakudalitsani m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani,

9 Yehova adzakukhazikirani yekha mtundu wa anthu wopatulika, monga anakulumbirirani; ngati mudzasunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi kuyenda m'njira zace.

10 Ndipo anthu onse a pa dziko lapansi adzaona kuti akuchulani dzina la Yehova; nadzakuopani.

11 Ndipo Yehova adzakucurukitsirani zokoma, m'zipatso za thupi lanu, ndi m'zipatso za zoweta zanu, ndi m'zipatso za nthaka yanu, m'dziko limene Yehova analumbirira makolo anu kuti adzakupatsani ilo,

12 Yehova adzakutsegulirani cuma cace cokoma, ndico thambo la kumwamba, kupatsa dziko lanu mvula m'nyengo yace, ndi kudalitsa nchito zonae za dzanja lanu; ndipo mudza kongoletsa amitundu ambiri, osakongola nokha.

13 Ndipo Yehova adzakuyesani mutu, si mcira ai; ndipo mudzakhala wa pamwamba pokha, si wapansi ai; ngati mudzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu, amene ndikuuzani lero, kuwasunga ndi kuwacita;

14 osapatukira mau ali onse ndikuuzani lero, kulamanja, kapena kulamanzere, kutsata milungu yina kuitumikira.

15 Koma kudzali, mukapanda kumvera mau a Yehova Mulungu wanu, kusamalira kucita malamulo ace onse ndi malemba ace amene ndikuuzani lero, kuti matemberero awa onse adzakugwerani ndi kukupezani,

16 Mudzakhala otembereredwa m'mudzi, ndi otembereredwa pabwalo.

17 Zidzakhala zotembereredwa mtanga wanu ndi coumbiramo mkate wanu.

18 Zidzakhala zotembereredwa zipatso za thupi lanu, ndi zipatso za nthaka yanu, zoswana za ng'ombe zanu, ndi zoswana za nkhosa zanu.

19 Mudzakhala otembereredwa polowa inu, ndi otembereredwa poturuka inu.

20 Yehova adzakutumizirani temberero, cisokonezeko, ndi kudzudzula monsemo mukaturutsa dzanja lanu kucita kanthu, kufikira mwaonongeka, kufikira mwatayika rosanga, cifukwa ca zocita inu zoipa, zimene wandisiya nazo,

21 Yehova adzakumamatiritsani mliri kufikira akakuthani kukucotsani kudziko, kumene mupitako kulilandira.

22 Yehova adzakukanthani ndi nthenda yoondetsa ya cifuwa, ndi malungo, ndi cibayo, ndi kutentha thupi, ndi lupanga, cinsikwi ndi cinoni; ndipo zidzakutsatani kufikira mwatayika.

23 Ndipo thambo lanu la pamwamba pamutu panu lidzakhala ngati mkuwa, ndi dziko liri pansi panu ngati citsulo.

24 Yehova adzasanduliza mvula ya dziko lanu ikhale pfumbi ndi phulusa; zidzakutsikirani kucokera kumwamba, kufikira mwaonongeka.

25 Yehova adzalola adani anu akukantheni; mudzawaturukira njira imodzi, koma mudzawathawa pamaso pao njira zisanu ndi ziwiri, ndipo mudzagwedezeka pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.

26 Ndipo mitembo yanu idzakhalacakudya ca mbalame zonse za m'mlengalenga, ndi zirombo zonse za pa dziko lapansi, ndipo palibe wakuziingitsa.

27 Yehova adzakukanthani ndi zirombo za ku Aigupto, ndi nthenda yoturuka mudzi, ndi cipere, ndi mphere, osacira nazo.

28 Yehova adzakukanthani ndi misala, ndi khungu, ndi kuzizwa mumtima;

29 ndipo mudzafufuza usana, monga wakhungu amafufuza mumdima, ndipo simudzapindula nazo njira zanu; koma mudzakhala wopsinjika, nadzakuberani masiku onse, wopanda wina wakukupulumutsani.

30 Mudzaparana ubwenzi ndi mkazi, koma mwamuna wina adzagona naye; mudzamanga nyumba, osakhala m'mwemo; mudzanka munda wamphesa, osalawa zipatso zace.

31 Adzapha ng'ombe yanu pamaso panu, osadyako inu; adzalanda buru wanu molimbana pamaso panu, osakubwezerani; adzapereka nkhosa zanu kwa adani anu, wopanda wina wakukupulumutsani.

32 Adzapereka ana anu amuna ndi akazi kwa anthu a mtundu wina, ndipo m'maso mwanu mudzada ndi kupenyerera, powalirira tsiku lonse; koma mulibe mphamvu m'dzanja lanu.

33 Mtundu wa anthu umene simudziwa udzadya zipatso za nthaka yanu ndi nchito zanu zonse; ndipo mudzakhala wopsinjika ndi wophwanyika masiku onse;

34 nimudzakhala oyeruka cifukwa comwe muciona ndi maso anu,

35 Yehova adzakukanthani ndi cironda coipa cosacira naco kumaondo, ndi kumiyendo, kuyambira pansi pa phazi lanu kufikira pamwamba pa mutu panu.

36 Yehova adzamukitsa inu, ndi mfumu yanu imene mudzadziikira, kwa mtundu wa anthu umene simudziwa, inu kapena makolo anu; ndipo mudzatumikirako milungu yina ya mitengo ndi miyala.

37 Ndipo mudzakhala codabwitsa, ndi nkhani, ndi nthanthi, mwa mitundu yonse ya anthu amene Yehova akutsogoleraniko.

38 Mudzaturuka nazo mbeu zambiri kumunda, koma mudzakolola pang'ono; popeza dzombe lidzazitha.

39 Mudzanka m'minda yamphesa ndi kuilima, koma osamwa vinyo wace, kapena kuchera mphesa zace, popeza citsenda cidzaidya.

40 Mudzakhala nayo mitengo yaazitona m'malire anu onset osadzola mafuta; popeza zipatso za mitengo yaazitona zidzapululuka.

41 Mudzabala ana amuna ndi akazi, osakhala nao, popeza adzalowa ukapolo.

42 Mitengo yanu yonse ndi zipatso za nthaka yanu zidzakhala zao zao za dzombe.

43 Mlendo wokhala pakati panu adzakulira-kulira inu, koma inu mudzacepera-cepera.

44 Iye adzakukongoletsani, osamkongoletsa ndinu; iye adzakhala mutu, koma inu ndinu mcira.

45 Ndipo matemberero awa onse adzakugwerani, nadzakulondolani, ndi kukupezani, kufikira mwaonongeka, popeza simunamvera mau a Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ace ndi malemba ace amene anakulamulirani;

46 ndipo zidzakukhalirani inu ndi mbeu zanu ngati cizindikilo ndi cozizwa, nthawi zonse.

47 Popeza simunatumikira Yehova Mulungu wanu ndi cimwemwe ndi mokondwera mtima, cifukwa ca kucuruka zinthu zonse;

48 cifukwa cace mudzatumikira adani anu amene Yehova adzakutumizirani, ndi njala, ndi ludzu, ndi usiwa, ndi kusowa zinthu zonse; ndipo adzaika goli lacitsulo pakhosi panu, kufikira atakuonongani.

49 Yehova adzakutengerani mtundu wa anthu wocokera kutali ku malekezero a dziko lapansi, monga iuluka mphungu; mtundu wa anthu amene simunamva malankhulidwe ao;

50 mtundu wa anthu wa nkhope yaukali, wosamalira nkhope ya wokalamba, wosamcitira cifundo mwana;

51 ndipo adzadya zipatso za ng'ombe zanu, ndi zipatso za nthaka yanu, kufikira mwaonongeka; osakusiyirani tirigu, vinyo, kapena mafuta, zoswana ng'ombe zanu, zoswana nkhosa zanu, kufikira atakuonongani.

52 Ndipo adzakuzingani m'midzi mwanu monse, kufikira adagwa malinga anu atali ndi olimba, amene munawakhulupirira, m'dziko lanu lonse; inde, adzakuzingani m'midzi mwanu monse, m'dziko lanu lonse limene Yehova Mulungu wanu akupatsani.

53 Ndipo mudzadya cipatso ca thupi lanu, nyama ya ana anu amuna ndi akazi amene Yehova Mulungu wanu anakupatsani; pakukumangirani tsasa ndi kukupsinjani adani anu.

54 Mwamuna wololopoka nkhongono ndi wanyonga pakati pa inu diso lace lidzaipira mbale wace, ndi mkazi wa pa mtima wace, ndi ana ace otsalira;

55 osapatsako mmodzi yense wa iwowa nyama ya ana ace alinkudyayo, popeza sikamtsalira kanthu; pakukumangirani tsasa ndi kukupsinjani mdani wanu m'midzi mwanu monse.

56 Mkazi wololopoka nkhongono ndi wanyonga pakati pa inu, wosayesa kuponda pansi ndi phazi lace popeza ndiye wanyonga, ndi wololopoka nkhongono, diso lace lidzamuipira mwamuna wa pamtima pace, ndi mwana wace wamwamuna ndi wamkazi;

57 ndico dfukwa ca matenda akuturuka pakati pa mapazi ace, ndi ana ace adzawabala; popeza adzawadya m'tseri posowa zinthu zonse; pakukumangirani tsasa ndi kukupsinjani mdaniwanu m'midzi mwanu.

58 Mukapanda kusamalira kucita mau onse a cilamulo ici olembedwa m'buku ili, kuopa dzina ili la ulemerero ndi loopsa, ndilo YEHOVA MULUNGU ANU;

59 Yehova adzacita miliri yanu ndi ya ana anu ikhale yodabwiza, miliri yaikuru ndi yokhalitsa, ndi nthenda zoipa ndi zokhalitsa.

60 Ndipo adzakubwezerani nthenda zonse za Aigupto, zimene munaziopa; ndipo zidzakumamatirani inu.

61 Ndiponso nthenda zonse ndi miliri yonse zosalembedwa m'buku la cilamulo ici, Yehova adzakutengerani izi, kufikira mwaonongeka.

62 Ndipo mudzatsala anthu pang'ono, mungakhale mukacuruka ngati nyenyezi za m'mwamba; popeza simunamvera mau a Yehova Mulungu wanu.

63 Ndipo kudzali kuti, monga Yehova anakondwera nanu kukucitirani zabwino, ndi kukucurukitsani; momwemo Yehova adzakondwera nanu kutayikitsa ndi kuononga inu, ndipo adzakuzulani kudziko kumene mulowako kulilandira.

64 Ndipo Yehova adzakubalalitsani mwa mitundu yonse ya anthu, kuyambira malekezero a dziko lapansi kufikira malekezero a dziko lapansi; ndipo kumeneko mudzatumikira milungu yina, imene simunaidziwa, inu ndi makolo anu, yamitengo ndi yamiyala.

65 Ndipo mwa a mitundu iyi simudzapumula, inde sipadzakhala popumulira phazi lanu; koma Yehova adzakupatsani kumeneko mtima wonjenjemera, m'maso mwanu mudzada, mudzafa ndi kulefuka mtima.

66 Ndipo moyo wanu udzakhala wanjiranjira pamaso panu, ndipo mudzacita mantha usiku ndi usana, osakhazika mtima za moyo wanu.

67 M'mawa mudzati, Mwenzi atafika madzulo! ndi madzulo mudzati, Mwenzi utafika m'mawa! cifukwa ca mantha a m'mtima mwanu amene mudzaopa nao, ndi cifukwa ca zopenya maso anu zimene mudzazipenya.

68 Ndipo Yehova adzakubwezerani ku Aigupto ndi ngalawa, pa njira imene ndinati kwa inu, kuti, Simudzaionanso; ndipo kumeneko mudzadzigulitsa kwa adani anu mukhale akapolo ndi adzakazi; koma palibe wogulainu.

29

1 Awa ndi mau a cipangano cimene Yehova analamulira Mose acicite ndi ana a Israyeli m'dziko la Moabu, pamodzi ndi cipanganoco anacita nao m'Horebe.

2 Ndipo Mose anaitana Israyeli wonse, nati nao, Munapenya inu zonse zimene Yehova anacitira Farao, ndi anyamata ace onse, ndi dziko lace lonse, pamaso panu m'dziko la Aigupto;

3 mayesero akuruwa maso anu anawapenya, zizindikilozo, ndi zozizwa zazikuru zija;

4 koma Yehova sanakupatsani mtima wakudziwa, ndi maso akupenya, ndi makutu akumva, kufikira lero lino.

5 Ndipo ndinakutsogolerani zaka makumi anai m'cipululu; zobvala zanu sizinatha pathupi panu, ndi nsapato zanu sizinatha pa phazi lanu.

6 Simunadya mkate, simunamwa vinyo kapena cakumwa colimba; kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

7 Ndipo pamene munafika pamalo pano, Sihoni mfumu ya Hesiboni, ndi Ogi mfumu ya Basana, anaturuka kudzakomana nafe kunkhondo, ndipo tinawakantha;

8 ndipo tinalanda dziko lao, ndi kulipereka likhale colowa cao ca Arubeni, ndi Agadi, ndi pfuko la hafu la Manase.

9 Cifukwa cace sungani mau a cipangano ici ndi kuwacita, kuti mucite mwanzeru m'zonse muzicita.

10 Muimirira inu nonse lero lino pamaso pa Yehova Mulungu wanu; mafumu anu, mapfuko anu, akuru anu, ndi akapitao anu, amuna onse a Israyeli;

11 makanda anu, akazi anu, ndi mlendo wanu wakukhala pakati pa zigono zanu, kuyambira wotema nkhuni kufikira wotunga madzi;

12 kuti mulowe cipangano ca Yehova Mulungu wanu, ndi lumbiriro lace, limene Yehova Mulungu wanu acita ndi inu lero lino;

13 kuti adzikhazikire inu, mtundu wace wa anthu lero lino, ndi kuti akhale kwa inu Mulungu, monga ananena ndi inu, ndi monga analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isake, ndi Yakobo.

14 Koma sindicita cipangano ici ndi lumbiro ili ndi inu nokha;

15 komanso ndi iye wakuimirira pano nafe lero lino pamaso pa Yehova Mulungu wathu, ndiponso ndi iye wosakhala pano nafe lero lino.

16 Pakuti mudziwa cikhalidwe cathu m'dziko la Aigupto, ndi kuti tinapyola pakati pa amitundu amene munawapyola;

17 ndipo munapenya zonyansa zao, ndi mafano ao, mtengo ndi mwala, siliva ndi golidi, zokhala pakati pao;

18 kuti angakhale pakati pa inu mwamuna, kapena mkazi, kapena banja, kapena pfuko, mtima wao watembenuka kusiyana naye Yehova Mulungu wathu lero lino, kuti apite ndi kutumikira milungu ya amitundu aja; kuti ungakhale pakati pa inu muzu wakubala ndulu ndi cowawa.

19 Ndipo kungakhale, akamva mau a lumbiro ili adzadzidalitsa m'mtima mwace, ndi kuti, Ndidzakhala nao mtendere, ndingakhale ndiyenda nao mtima wanga wopulukira, kuledzera nditamva ludzu;

20 Yehova sadzamkhululukira, koma pamenepo mkwiyo wa Yehova ndi nsanje yace zidzamfukira munthuyo; ndipo temberero lonse lolembedwa m'buku ili lidzamkhalira; ndipo Yehova adzafafaniza dzina lace pansi pa thambo.

21 Ndipo Yehova adzamsiyanitsa ndi mafuko onse a Israyeli ndi kumcitira coipa, monga mwa matemberero onse a cipangano colembedwa m'buku ili la cilamulo.

22 Ndipo mbadwo ukudza, ana anu akuuka mutafa inu, ndi mlendo wocokera ku dziko lakutali, adzati, pakuona iwo miliri ya dziko ili, ndi nthendazi; Yehova awadwalitsa nazo,

23 ndi kuti lidapsa dziko lace lonse ndi sulfure, ndi mcere, kuti sabzalamo, kapena siliphukitsa kanthu kapena sumerapo msipu, monga kupasula kwace kwa Sodomu ndi Gomora, Adima, ndi Zeboimu, imene Yehova anaipasula m'mkwiyo wace ndi ukali wace;

24 inde amitundu onse adzati, Yehova anacitira dziko ili cotero cifukwa ninji? nciani kupsa mtima kwakukuru kumene?

25 Pamenepo adzati, Popeza analeka cipangano ca Yehova, Mulungu wa makolo ao, cimene anacita nao pakuwaturutsa m'dziko la Aigupto;

26 napita natumikira milungu yina, naigwadira, milungu imene sanaidziwa, imene sanawagawira;

27 cifukwa cace Mulungu anapsera mtima dziko ili kulitengera temberero lonse lolembedwa m'buku ili.

28 Ndipo Yehova anawazula m'nthaka mwao mokwiya ndi mozaza, ndi m'ukali waukuru, nawaponya m'dziko lina, monga lero lino.

29 Zinsinsi nza Yehova Mulungu wathu; koma zobvumbuluka nza ife ndi ana athu kosatha, kuti ticite mau onse a cilamulo ici.

30

1 Ndipo kudzakhala, zikakugwerani zonsezi, mdalitso ndi temberero, ndinaikazi pamaso panu, ndipo mukazikumbukila mumtima mwanu mwa amitundu onse, amene Yehova Mulungu wanu anakupitikitsiraniko;

2 nimukabwerera kwa Yehova Mulungu wanu, ndi kumvera mali ace, monga mwa zonse ndikuuzani lero lino, inu ndi ana anu, ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse;

3 pamenepo Yehova Mulungu wanu adzaucotsa ukapolo wanu, ndi kukucitirani cifundo; nadzabwera ndi kukumemezani mwa mitundu yonse ya anthu, kumene Yehova Mulungu wanu anakubalalitsiraniko.

4 Otayika anu akakhala ku malekezero a thambo, Yehova Mulungu wanu adzakumemezani kumeneko, nadzakutenganiko;

5 ndipo Yehova Mulungu wanu adzakulowetsani m'dziko lidakhala lao lao la makolo anu, nilidzakhala lanu lanu; ndipo adzakucitirani zokoma, ndi kukucurukitsani koposa makolo anu.

6 Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudulani mtima wanu ndi mtima wa mbeu zanu, kuti mukonde Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, kuti mukhale ndi moyo.

7 Ndipo Yehova Mulungu wanu adzaika matemberero awa onse pa adani anu, ndi iwo akukwiya ndi inu, amene anakulondolani.

8 Pamenepo mutembenuke ndi kumvera mau a Yehova, ndi kucita malamulo ace onse amene ndikuuzani lero lino.

9 Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakucurukitsirani nchito zonse za dzanja lanu, zipatso za thupi lanu, ndi zipatso za zoweta zanu, ndi zipatso za nthaka yanu, zikukomereni; popeza Yehova Mulungu wanu adzakondweranso kukucitirani zokoma; monga anakondwera ndi makolo anu;

10 ngati mudzamvera mau a Yehova Mulungu wanu, kuwasunga malamulo ace ndi malemba ace olembedwa m'buku la cilamulo ici; ngati mudzabwerera kudza kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse.

11 Pakuti lamulo ili ndikuuzani lero lino, silikulakani kulizindikira, kapena silikhala kutali.

12 Silikhala m'mwamba, kuti mukati, Adzatikwerera m'mwamba ndani, ndi kubwera nalo kwa ife, ndi kutimvetsa ili, kuti tilicite?

13 Ndipo silikhala tsidya la nyanja, kuti mukati, Adzatiolokera ndani tsidya la nyanja, ndi kutitengera ili, ndi kutimvetsa ili, kuti tilicite?

14 Pakuti mauwa ali pafupifupi ndi inu, m'kamwa mwanu, ndi m'mtima mwanu, kuwacita.

15 Tapenyani, ndaika pamaso panu lero lino moyo ndi zokoma, imfa ndi zoipa;

16 popeza ndikuuzani lero kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda m'njira zace, ndi kusunga malamulo ace ndi malemba ace ndi maweruzo ace, kuti mukakhale ndi moyo ndi kucuruka, ndi kuti Yehova Mulungu wanu akakudalitseni m'dziko limene mulowako kulilandira.

17 Koma mukatembenukira mtima wanu, osamvera inu, nimukaceteka, ndi kugwadira milungu yina ndi kuitumikira;

18 ndikulalikirani inu lero, kuti mudzatayika ndithu, masiku anu sadzacuruka m'dziko limene muolokera Yordano kulowamo kulilandira.

19 Ndicititsa mboni lero kumwamba ndi dziko lapansi zitsutse inu; ndaika pamaso panu moyo ndi imfa, mdalitso ndi temberero; potero, sankhani moyo, kuti mukhale ndi moyo, inu ndi mbeu zanu;

20 kukonda Yehova Mulungu wanu, kumvera mau ace, ndi kummamatira iye, tr pakuti iye ndiye moyo wanu, ndi masiku anu ocuruka; kuti mukhale m'dziko limene Yehova analumbirira makolo anu, Abrahamu, Isake, ndi Yakobo, kuwapatsa ili.

31

1 Ndipo Mose anamuka nanena mau awa kwa Israyeli wonse,

2 nati nao, Ndine munthu wa zaka zana ndi makumi awiri lero lino; sindikhozanso kuturuka ndi kulowa ndipo Yehova anati kwa ine, Sudzaoloka Yordano uyu.

3 Yehova Mulungu wanu ndiye adzaoloka pamaso panu, iye ndiye adzaononga amitundu awo pamaso panu, ndipo mudzawalandira. Yoswa ndiye adzakutsogolerani pooloka, monga ananena Yehova.

4 Ndipo Yehova adzawacitira monga anacitira Sihoni ndi Ogi, mafumu a Aamori, ndi dziko lao limene analiononga.

5 Yehova akadzawapereka pamaso panu, muziwacitira monga mwa lamulo lonse ndakuuzani.

6 Khalani amphamvu, limbikani mitima, musamacita mantha, kapena kuopsedwa cifukwa ca iwowa; popeza Yehova Mulungu wanu ndiye amene amuka nanu; iye sadzakusowani, kapena irukusiyani.

7 Ndipo Mose anaitana Yoswa, nati naye pamaso pa Israyeli wonse, Khala wamphamvu, nulimbe mtima; pakuti udzalowa nao anthu awa m'dziko limene Yehova analumbirira makolo ao kuwapatsa ilo; ndipo iwe udzawalandiritsa ilo.

8 Ndipo Yehova, iye ndiye amene akutsogolera; iye adzakhala ndi iwe, iye sadzakusowa kapena kukusiya; usamacita mantha, usamatenga nkhawa.

9 Ndipo Mose analembera cilamulo ici, nacipereka kwa ansembe, ana a Levi, akunyamula likasa la cipangano la Yehova, ndi kwa akuru onse a Israyeli,

10 Ndipo Mose anawauza, ndi kuti, Pakutha pace pa zaka zisanu ndi ziwiri, pa nyengo yoikika ya m'caka cakulekerera, pa madyerero a misasa;

11 pakufika Israyeli wonse kuoneka pamaso pa Yehova Mulungu wanu, m'malo amene adzasankha, muzilalikira cilamulo ici pamaso pa Israyeli wonse, m'makutu mwao.

12 Sonkhanitsan; anthu, amuna ndi akazi ndi ana ang'ono, ndi mlendo wokhala m'midzi mwanu, kuti amve, ndi kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu, ndi kusamalira kucita mau onse a cilamulo ici;

13 ndi kuti ana ao osadziwa amve, oaphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu, masiku onse akukhala ndi moyo inu kudziko kumene muolokera Yordano kulilandira likhale lanu lanu.

14 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Taona, ayandikira masiku ako akuti uyenera kufa; kaitane Yoswa, nimuoneke m'cihema cokomanako, kuti ndimlangize. Namuka Mose ndi Yoswa, naoneka m'cihema cokomanako.

15 Ndipo Yehova anaoneka m'cihema, m'mtambo njo; ndipo mtambo njo unaima pa khomo la cihema.

16 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Taona, udzagona tulo ndi makolo ako; ndi anthu awa adzauka, oadzatsata ndi cigololo milungu yacilendo ya dziko limene analowa pakati pace, nadzanditava Ine, ndi kutyola cipangano canga ndinapangana naoco.

17 Pamenepo ndidzawapsera mtima tsiku ilo, ndipo ndidzawataya, ndi kuwabisira nkhope yanga, ndipo adzathedwa, ndi zoipa ndi zobvuta zambiri zidzawafikira; kotero kuti adzati tsiku lija, Sizitifikira kodi zoipa izi popeza Mulungu wathu sakhala pakati pa ife?

18 Koma Ine ndidzabisatu nkhope yanga tsiku lija cifukwa ca zoipa zonse adazicita; popeza anadzitembenukira milungu yina.

19 Ndipo tsopano mudzilemberere nyimbo iyi, ndi kuphunzitsa ana a Israyeli iyi: mulike m'kamwa mwao, kuti nyimbo iyi indicitire mboni yotsutsa ana a Israyeli.

20 Pakuti nditakalowetsa awa m'dziko limene ndinalumbirira makolo ao, moyenda mkaka ndi uci ngati madzi; ndipo atadya nakhuta, nanenepa, pamenepo adzatembenukira milungu yina, ndi kuitumikira, ndi kundipeputsa Ine, ndi kutyola cipangano canga.

21 Ndipo kudzakhala, zitawafikira zoipa ndi zobvuta zambiri, nyimbo iyi idzacita mboni pamaso pao; popeza siidzaiwalika m'kamwa mwa mbeu zao; popeza ndidziwa zolingirira zao azicita lero lino, ndisanawalowetse m'dziko limene ndinalumbira.

22 Potero Mose analembera nyimboyi tsiku lomweli, naiphunzitsa ana a Israyeli.

23 Ndipo anauza Yoswa mwana wa Nuni, nati, Khala wamphamvu, nulimbe mtima; pakuti udzalowa nao ana a Israyeli m'dziko limene ndinawalumbirira: ndipo Ine ndidzakhala ndi iwe.

24 Ndipo kunali, Mose atatha kulembera mau a cilamulo ici m'buku, kufikira atalembera onse,

25 Mose anauza Alevi akunyamula likasa la cipangano la Yehova, ndi kuti,

26 Landirani buku ili la cilamulo, nimuliike pambali pa likasa la cipangano la Yehova Mulungu wanu, likhale komweko mboni yakutsutsa inu.

27 Pakuti ndidziwa kupikisana kwanu, ndi kupulukira kwanu; taonani, pokhala ndikali ndi moyo pamodzi ndi inu lero, mwapikisana ndi Yehova: koposa kotani nanga nditamwalira ine!

28 Ndisonkhanitsire akuru onse a mapfuko anu, ndi akapitao anu, kuti ndinene mau awa m'makutu mwao, ndi kucititsa mboni kumwamba ndi dziko lapansi zitsutse iwo.

29 Pakuti ndidziwa kuti nditamwalira ine mudzadziipsa ndithu, ndi kupatuka m'njira imene ndinakuuzani; ndipo cidzakugwerani coipa masiku otsiriza; popeza mudzacita coipa pamaso pa Yehova, kuutsa mkwiyo wace ndi nchito za manja anu.

30 Ndipo Mose ananena mau a nyimbo iyi m'makutu mwa msonkhano wonse wa Israyeli, kufikira adatha.

32

1 Kumwamba kuchere khutu, ndipo ndidzanena; Ndi dziko lapansi limve mau a m'kamwa mwanga;

2 Ciphunzitso canga cikhale ngati mvula; Maneno anga agwe ngati mame; Ngati mvula yowaza pamsipu, Ndi monga madontho a mvula pazitsamba.

3 Pakuti ndidzalalika dzina la Yehova; Nenani kuti Mulungu wathu ndi wamkulu.

4 Thanthwe, nchito yace ndi yangwiro; Pakuti njira zace zonse ndi ciweruzo; Mulungu wokhulupirika ndi wopanda cisalungamo; Iye ndiye wolungama ndi wolunjika,

5 Anamcitira zobvunda si ndiwo ana ace, cirema ncao; Iwo ndiwo mbadwo wopulukira ndi wokhotakhota.

6 Kodi mubwezera Yehova cotero, Anthu inu opusa ndi opanda nzeru? Kodi si ndiye Atate wanu, Mbuyewanu; Anakulengani, nakukhazikitsani?

7 Kumbukirani masiku akale, Zindikirani zaka za mibadwo yambiri; Funsani atate wanu, adzakufotokozerani; Akuru anu, adzakuuzani.

8 Pamene Wam'mwambamwamba anagawira amitundu colowacao, Pamene anagawa ana a anthu, Anaika malire a mitundu ya anthu, Monga mwa kuwerenga kwao kwa ana a Israyeli,

9 Pakuti gawo la Yehova ndilo anthu ace; Yakobo ndiye muyeso wa colowacace.

10 Anampeza m'dziko la mabwinja, ndi m'cipululu colira copanda kanthu; Anamzinga, anamlangiza, Anamsunga ngati kamwana lea m'diso;

11 Monga mphungu ikasula cisa cace, Nikapakapa pa ana ace, Iye anayala mapiko ace, nawalandira, Nawanyamula pa mapiko ace;

12 Yehova yekha anamtsogolera, Ndipo palibe mulungu wacilendo naye.

13 Anamuyendetsa pa misanje ya dziko lapansi, Ndipo anadya zipatso za m'minda; Namyamwitsa uci wa m'thanthwe, Ndi mafutam'mwala wansangalabwe;

14 Mafuta a mkaka wang'ombe, ndi mkaka wankhosa, Ndi mafuta a ana a nkhosa, Ndi nkhosa zamphongo za mtundu wa ku Basana, ndi atonde, Ndi imso zonenepa zatirigu; Ndipo munamwa vinyo, mwazi wamphesa,

15 Koma Yesuruni anasanduka wonenepa, natazira; Wasanduka wonenepa, wakula, wakuta ndi mafuta; Pamenepo anasiya Mulungu amene anamlenga, Napeputsa thanthwe la cipulumutso cace.

16 Anamcititsa nsanje ndi milungu yacilendo, Anautsa mkwiyo wace ndi zonyansa.

17 Anaziphera nsembe ziwanda, si ndizo Mulungu ai; Milungu yosadziwa iwo, Yatsopano yofuma pafupi, Imene makolo anu sanaiopa,

18 Mwaleka Thanthwe limene linakubalani, Mwaiwala Mulungu amene anakulengani.

19 Ndipo Yehova anaciona, nawanyoza, Pakuipidwa nao ana ace amuna, ndi akazi.

20 Ndipo iye anati, Ndidzawabisira nkhope yanga, Ndidzaona kutsiriza kwao; Popeza iwo ndiwo mbadwo wopulukira, Ana osakhulupirika iwo.

21 Anautsa nsanje yanga ndi cinthu cosati Mulungu; Anautsa mkwiyo wanga om zopanda pace zao. Ndidzautsa nsanje yao ndi iwo osakhala mtundu wa anthu; Ndidzautsa mkwiyo wao ndi mtundu wa anthu opusa.

22 Pakuti wayaka moto mu mkwiyo wanga, Utentha kumanda kunsi Ukutha dziko lapansi ndi zipatso zace Nuyatsa maziko a mapiri,

23 Ndidzawaunjikira zoipa; Ndidzawathera nubvi yanga.

24 Adzaonda nayo njala Adzanyekeka ndi makala a moto, cionongeko cowawa; Ndipo ndidzawatumizira mana a zirombo, Ndi ululu wa zokwawa m'pfumbi.

25 Pabwalo lupanga lidzalanda, Ndi m'zipinda mantha; Lidzaononga mnyamata ndi namwali, Woyamwa pamodzi ndi munthu waimvi.

26 Ndinati, Ndikadawauzira ndithu, Ndikadafafaniza cikumbukiro cao mwa anthu;

27 Ndikadapanda kuopa mkwiyo wapamdani, Angayese molakwa outsana nao, Anganene, Lakwezeka dzanja lathu, Ndipo Yehova sanacita ici conse.

28 Popeza iwo ndiwo mtundu wa anthu wosowa uphungu konse, Ndipo alibe cidziwitso.

29 Akadakhala nazo nzeru, akadazindikira ici, Akadasamalira citsirizo cao!

30 Mmodzi akadapitikitsa zikwi, Awiri akadathawitsa zikwi khumi, Akadapanda kuwagulitsa Thanthwelao, Akadapanda kuwapereka Yehova.

31 Popeza thanthwe lao nlosanga Thanthwe lathu, Oweruza a pamenepo ndiwo adani athu.

32 Pakuti mpesa wao ndiwo wa ku Sodomu, Ndi wa m'minda ya ku Gomora; Mphesa zao ndizo mphesa zandulu, Matsangwi ao ngowawa.

33 Vinyo wao ndiwo ululu wa zinjoka, Ndi ululu waukali wa mphiri.

34 Kodi sicisungika ndi Ine, Colembedwa cizindikilo mwa cuma canga ceni ceni?

35 Kubwezera cilango nkwanga, kubwezera komwe, Pa nyengo ya kuterereka phazi lao; Pakuti tsiku la tsoka lao layandika, Ndi zinthu zowakonzeratu zifulomira kudza.

36 Popeza Yehova adzaweruza anthuace, Nadzacitira nsoni anthu ace; Pakuona iye kuti mphamvu yao yatha, Wosatsala womangika kapena waufulu,

37 Pamenepo adzati, Iri kuti milunguyao, Thanthwe limene anathawirako?

38 Imene inadya mafuta a nsembe zao zophera, Nimwa vinyo wa nsembe yao yothira? Iuke nikuthandizeni, Ikhale pobisalapo panu.

39 Tapenyani tsopano kuti Ine ndine iye, Ndipo palibe mulungu koma Ine; Ndipha Ine, ndikhalitsanso ndi mayo: Ndikantha, ndicizanso Ine; Ndipo palibe wakulanditsa m'dzanja langa.

40 Pakuti ndikweza dzanja langa kuloza kumwamba, Ndipo nditi, Pali moyo wanga kosatha,

41 Ndikanola lupanga langa lonyezimira, Ndi dzanja langa likagwira ciweruzo; Ndidzabwezera cilango ondiukira, Ndi kulanga ondida.

42 Mibvi yanga ndiiledzeretsa nao mwazi, Ndi lupanga langa lidzalusira nyama; Ndi mwazi wa ophedwa ndi ogwidwa, Ndi mutu wacitsitsi wa mdani,

43 Kondwerani, amitundu inu, ndi anthu ace; Adzalipsira mwazi wa atumiki ace, Adzabwezera cilango akumuukira, Nadzafafanizira zoipa dziko lace, ndi anthu ace.

44 Ndipo anadza Mose nanena mau onse a nyimbo iyi m'makutu mwa anthu, iye, ndi Hoseya mwana wa Nuni.

45 Ndipo Mose anatha kunena mau awa onse kwa Israyeli wonse;

46 nati nao, Ikani mitima yanu pa mau onse ndikucitirani nao mboni lero; kuti muuze ana anu asamalire kuwacita mau onse a cilamulo ici.

47 Pakuti sicikhala kwa inu cinthu copanda pace, popeza ndico moyo wanu, ndipo mwa cinthu ici mudzacurukitsa masiku anu m'dziko limene muolokera Yordano, kulilandira.

48 Ndipo Yehova ananena ndi Mose tsiku lomweli, ndi kuti,

49 Kwera m'phiri muno mwa Abarimu, phiri la Nebo, lokhala m'dziko la Moabu, popenyana ndi Yeriko; nupenye dziko la Kanani, limene ndipereka kwa ana a Israyeli likhale lao lao;

50 nufe m'phiri m'mene ukweramo, nuitanidwe kumka kwa anthu a mtundu wako; monga Aroni mbale wako anafa m'phiri la Hori, naitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wace;

51 popeza munandilakwira pakati pa ana a Israyeli ku madzi a Meriba wa Kadesi m'cipululu ca Zini, popeza simunandipatula Ine pakati pa ana a Israyeli,

52 Pakuti udzapenya dzikoli pandunji pako; koma osalowako ku dziko limene ndipatsa ana a Israyeli.

33

1 Ndipo mdalitso, Mose munthu wa Mulungu anadalitsa nao ana a Israyeli asanafe, ndi uwu.

2 Ndipo anati, Yehova anafuma ku Sinai, Nawaturukiraku Seiri; Anaoneka wowala pa phiri la Parana, Anafumira kwa opatulika zikwi zikwi; Ku dzanja lamanja lace kudawakhalira lamulo lamoto.

3 Inde akonda mitundu ya anthu; Opatulidwa ace onse ali m'dzanjamwanu; Ndipo akhala pansi ku mapazi anu; Yense adzalandirako mau anu.

4 Mose anatiuza cilamulo, Colowa ca msonkhano wa Yakobo.

5 Ndipo iye anali mfumu m'Yesuruni, Pakusonkhana mafumu a anthu, Pamodzi ndi mapfuko a Israyeli.

6 Rubeni akhale ndi moyo, asafe, Koma amuna ace akhale owerengeka.

7 Za Yuda ndi izi; ndipo anati, Imvani, Yehova, mau a Yuda, Ndipo mumfikitse kwa anthu ace; Manja ace amfikire; Ndipo mukhale inu thandizo lace pa iwo akumuukira.

8 Ndipo za Levi anati, Tumimu ndi Urimu wanu zikhala ndi wokondedwa wanu, Amene mudamuyesa m'Masa, Amene mudalimbana naye ku madzi a Meriba;

9 Amene anati za atate wace ndi amai wace, Sindinamuone; Sanazindikira abale ace, Sanadziwa ana ace omwe; Popeza anasamalira mau anu, Nasunga cipangano canu.

10 Adzaphunzitsa Yakobo maweruzo anu, Ndi Israyeli cilamulo canu; Adzaika cofukiza pamaso panu, Ndi nsembe yopsereza yamphumphu pa guwa la nsembe lanu.

11 Dalitsani, Yehova, mphamvu yace, Nimulandire nchito ya manja ace; Akantheni m'cuuno iwo akumuukira, Ndi iwo akumuda, kuti asaukenso.

12 Za Benjamini anati, Wokondedwa wa Yehova adzakhala ndi iye mokhazikika; Amphimba tsiku lonse, Inde akhalitsa pakati pa mapewa ace.

13 Ndipo za Yosefe anati, Yehova adalitse dziko lace; Ndi zinthu zofunikatu za m'mwamba, ndi mame, Ndi madzi okhala pansipo;

14 Ndi zipatso zofunikatu za dzuwa, Ndi zomera zofunikatu za mwezi,

15 Ndi zinthu zoposa za mapiri akale, Ndi zinthu zofunikatu za zitunda zosatha,

16 Ndi zinthu zofunikatu za dziko lapansi, ndi kudzala kwace, Ndi cibvomerezo ca iye anakhala m'citsambayo; Mdalitso ufike pa mutu wa Yosefe, Ndi pakati pa mutu wace wa iye wokhala padera ndi abale ace.

17 Woyamba kubadwa wa ng'ombe yace, ulemerero ndi wace; Nyanga zace ndizo nyanga zanjati; Adzatunga nazo mitundu ya anthu pamodzi, kufikira malekezero a dziko lapansi. Iwo ndiwo zikwi khumi za Efraimu, Iwo ndiwo zikwi za Manase.

18 Ndi za Zebuloni anati, Kondwera, Zebuloni, ndi kuturukakwako; Ndi Isakara, m'mahema mwako.

19 Adzaitana mitundu ya anthu afike kuphiri; Apo adzaphera nsembe za cilungamo; Popeza adzayamwa zocuruka za m'nyanja, Ndi cuma cobisika mumcenga.

20 Ndi za Gadi anati, Wodala iye amene akuza Gadi; Akhala ngati mkango waukazi, Namwetula dzanja, ndi pakati pa mutu pomwe.

21 Ndipo anadzisankhira gawo loyamba, Popeza kumeneko kudasungika gawo la wolamulira; Ndipo anadza ndi mafumu a anthu, Anacita cilungamo ca Yehova, Ndi maweruzo ace ndi Israyeli.

22 Ndi za Dani anati, Dani ndiye mwana wa mkango, Wakutumpha moturuka m'Basana.

23 Za Nafitali anati, Nafitali, wokhuta nazo zomkondweretsa, Wodzala ndi mdalitso wa Yehova; Landira kumadzulo ndi kumwela.

24 Ndi za Aseri anati, Aseri adalitsidwe mwa anawo; Akhale wobvomerezeka mwa abale ace, Abviike phazi lace m'mafuta.

25 Nsapato zako zikhale za citsulo ndi mkuwa; Ndipo monga masiku ako momwemo mphamvu yako.

26 Palibe wina ngati Mulungu, Yesuruni iwe, Wakuyenda wokwera pathambo, kukuthandiza, Ndi pa mitambo m'ukulu wace.

27 Mulungu wamuyaya ndiye mokhaliramo mwako; Ndi pansipo pali manja osatha. Ndipo aingitsa mdani pamaso pako, Nati, Ononga.

28 Ndipo Israyeli akhala mokhazikika pa yekha; Kasupe wa Yakobo; Akhala m'dziko la tirigu ndi vinyo; Inde thambo lace likukha mame.

29 Wodala iwe, Israyeli; Akunga iwe ndani, mtundu wa anthu opulumutsidwa ndi Yehova, Ndiye cikopa ca thandizo lako, Iye amene akhala lupanga la ukulu wako! Ndi adani ako adzakugonjera; Ndipo udzaponda pa misanje yao.

34

1 Ndipo Mose anakwera kucokera ku zidikha za Moabu, kumka ku phiri la Nebo, pamwamba pa Pisiga, popenyana ndi Yeriko. Ndipo Yehova anamuonetsa dziko lonse la Gileadi, kufikira ku Dani;

2 ndi Nafitali lonse, ndi dziko la Efraimu, ndi Manase, ndi dziko lonse la Yuda, kufikira nyanja ya m'tsogolo;

3 ndi kumwela, ndi cidikha eli cigwa ca Yeriko, mudzi wa migwalangwa, kufikira ku Zoari.

4 Ndipo Yehova anati kwa iye, Si ili dziko ndinalumbirira Abrahamu, Isake, ndi Yakobo, ndi kuti, Ndidzalipereka kwa mbeu zako. Ndinakuonetsa ili m'maso, koma sudzaolokako.

5 Ndipo Mose mtumiki wa Yehova anamwalirako m'dziko la Moabu, monga mwa mau a Yehova.

6 Ndipo iye anamuika m'cigwa m'dziko la Moabu popenyana ndi Beti-peori; koma palibe munthu wakudziwa kumanda kwace kufikira lero lino.

7 Ndipo zaka zace za Mose ndizo zana limodzi ndi makumi awiri, pakumwalira iye; diso lace silinacita mdima, ndi mphamvu yace siidaleka.

8 Ndipo ana a Israyeli analira Mose m'zidikha za Moabu masiku makumi atatu; potero anatha masiku akulira maliro a Mose.

9 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anadzala ndi mzimu wanzeru; popeza Mose adamuikira manja ace; ndi ana a Israyeli anamvera iye, nacita monga Yehova adauza Mose.

10 Ndipo sanaukanso mnereri m'lsrayeli ngati Mose, amene Yehova anadziwana naye popenyana maso;

11 kunena za zizindikilo ndi zozizwa zonse zimene Yehova anamtumiza kuzicita m'dziko la Aigupto kwa Farao, ndi anyamata ace onse, ndi dziko lace lonse;

12 ndi kunena za dzanja la mphamvu lonse, ndi coopsa cacikuru conse, cimene Mose anacita pamaso pa Israyeli wonse.