1

1 NDIPO maina a ana a Israyeli, amene analowa m'Aigupto ndi Yakobo ndi awa, analowa munthu ndi banja lace:

2 Rubeni, Simeoni, Levi ndi Yuda;

3 Isakara, Zebuloni, ndi Benjamini;

4 Dani ndi Nafitali, Gadi ndi Aseri.

5 Ndipo amoyo onse amene anaturuka m'cuunomwace mwa Yakobo ndiwo makumi asanu ndi awiri; kama Yosefe anali m'Aigupto.

6 Ndipo anafa Yosefe, ndi abale ace onse, ndi mbadwo uwo wonse.

7 Ana a Israyeli ndipo anaswana, nabalana, nacuruka, nakhala nazo mphamvu zazikuru; ndipo dziko linadzala nao.

8 Pamenepo inalowa mfumu yatsopano m'ufumu wa Aigupto, imene siinadziwa Yosefe.

9 Ndipo ananena ndi anthu ace, Taonani, anthu, ndiwo ana a Israyeli, acuruka, natiposa mphamvu.

10 Tiyeni, tiwacenjerere angacuruke, ndi kuphatikizana ndi adani athu ikafika nkhondo, ndi kulimbana nafe, ndi kucoka m'dzikomo.

11 Potero anawaikira akuru a misonkho kuti awasautse ndi akatunduno. Ndipo anammangira Farao midzi yosungiramo cuma, ndiyo Pitomu ndi Ramese.

12 Koma monga momwe anawasautsiramo, momwemo anacuruka, momwemonso anafalikira. Ndipo anabvutika cifukwa ca ana a Israyeli.

13 Ndipo Aaigupto anawagwiritsa ana a Israyeli nchito yosautsa;

14 nawawitsa moyo wao ndi nchito yolimba, ya dothi ndi ya njerwa, ndi nchito zonse za pabwalo, nchito zao zonse zimene anawagwiritsa nzosautsa.

15 Ndipo mfumu ya Aigupto inanena ndi anamwino a Ahebri, dzina lace la wina ndiye Sifra, dzina la mnzace ndiye Puwa;

16 ninati, Pamene muciza akazi a Ahebri nimuwaone pamipando; akakhala mwana wamwamuna, mumuphe; akakhala wamkazi, akhale ndi moyo.

17 Koma anamwino anaopa Mulungu, ndipo sanacita monga mfumu ya Aigupto inawauza, koma analeka ana amuna akhale ndi moyo.

18 Ndipo mfumu ya Aigupto inaitana anamwino, ninena nao, Mwacita ici cifukwa ninji, ndi kuleka ana amunawo akhale ndi moyo?

19 Ndipo anamwino ananena ndi Farao, Popeza akazi a Ahebri safanana ndi akazi a Aigupto; pakuti ali ndi mphamvu, naona ana asanalike anamwino.

20 Potero Mulungu anawacitira zabwino anamwino; ndipo anthuwo anacuruka, nakhala nazo mphamvu zazikuru.

21 Ndipo kunatero kuti, popeza anamwino anaopa Mulungu, iye anawamangitsira mabanja.

22 Ndipo Farao analamulira anthu ace onse, ndi kuti, Ana amuna onse akabadwa aponyeni m'nyanja, koma ana akazi onse alekeni amovo.

2

1 Ndipo anamuka munthu wa banja la Levi, natenga mwana wamkazi wa Levi.

2 Ndipo anaima mkaziyo, naonamwanawamwamuna; m'mene anamuona kuti ali wokoma, anambisa miyezi itatu.

3 Koma pamene sanathe kumbisanso, anamtengera kabokosi kagumbwa, napakapo nkhunga ndi phula; naikamo mwanayo, nakaika pakati pa mabango m'mbali mwa nyanja.

4 Ndipo mlongo wace anaima patali, adziwe comwe adzamcitira.

5 Ndipo mwana wamkazi wa Farao anatsikira kukasamba m'nyanja; ndipo atsikana ace anayendayenda m'mbali mwa nyanja; ndipo iye anaona kabokosi pakati pa mabango, natuma mdzakazi wace akatenge.

6 Pamene anakabvundukula, anapenya mwanayo; ndipo, taonani, khandalo lirikulira. Ndipo anamva naye cifundo, nati, Uyu ndiye wa ana a Ahebri.

7 Pamenepo mlongo wace ananena ndi mwana wamkazi wa Farao, Ndipite ine kodi kukuitanirani woyamwitsa wa Ahebri, akuyamwitsireni mwanayo?

8 Ndipo mwana wamkazi wa Farao ananena naye, Pita. Napita namwaliyo, nakaitana amace wa mwanayo.

9 Ndipo mwana wamkazi wa Farao ananena naye, Pita naye mwana uyu, ndi kundiyamwitsira iye, ndidzakupatsa mphotho yako. Ndipo mkaziyo anatenga mwanayo, namyamwitsa,

10 Ndipo atakula mwanayo, anapita naye kwa mwana wamkazi wa Farao, ndipo iye anakhala mwana wace. Ndipo anamucha dzina lace Mose, nati, Cifukwa ndinambvuula m'madzi.

11 Ndipo kunali masiku amenewo, atakula Mose, kuti anaturukira kukazonda abale ace, napenya akatundu ao; ndipo anaona munthu M-aigupto ali kukantha Mhebri, wa abale ace.

12 Ndipo anaunguza kwina ndi kwina, ndipo pamene anaona kuti palibe munthu, anakantha M-aigupto, namfotsera mumcenga.

13 M'mawa mwace anaturukanso, ndipo, taonani, anthu awiri Ahebri alikugwirana; ndipo ananena ndi wocimwayo, kuti, Umpandiranji mnzako?

14 Koma anati, Wakuika iwe ndani ukhale mkuru ndi woweruza wathu? kuteroku ukuti undiphe, monga unamupha M-aigupto? Ndipo Mose anacita mantha, nanena, Ndithu cinthuci cadziwika.

15 Pamene Farao anacimva ici, anafuna kupha Mose. Koma Mose anathawa pankhope pa Farao, nakhala m'dziko la Midyani; nakhala pansi pacitsime.

16 Ndipo wansembe wa Midyani anali nao ana akazi asanu ndi awiri, amene anadza kudzatunga madzi; ndipo anadzaza mimweco kuti amwetse gulu la atate wao.

17 Pamenepo anadza abusa nawapitikitsa; koma Mose anauka nawathandiza, namwetsa gulu lao.

18 M'mene anafika kwa Rehueli atate wao, iye anati, Mwabwera msanga bwanji lero?

19 Ndipo anati two, Munthu M-aigupto anatilanditsa m'manja a abusa, natitungiranso madzi okwanira, namwetsa gululi.

20 Ndipo anati kwa ana ace akazi, Ali kuti iye? Mwamsiyiranji munthuyo? Kamuitaneni, adzadye cakudya.

21 Ndipo Mose anabvomera kukhala naye munthuyo; ndipo anampatsa Mose mwana wace wamkazi Zipora.

22 Ndipo anaona mwana, ndi Mose anamucha dzina lace Gerisomu; pakuti anati, Ndakhala mlendo m'dziko la eni.

23 Ndipo kunali pakupita masiku ambiri aja, idafa mfumu ya Aigupto; ndi ana a Israyeli anatsitsa moyo cifukwa ca ukapolo wao, nalira, ndi kulira kwao kunakwera kwa Mulungucifukwa ca ukapolowo.

24 Ndipo Molungu anamva kubuula kwao, ndi Mulungu anakumbukila cipangano cace ndi Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo.

25 Ndipo Molungu anapenya Aisrayeli, ndi Mulungu anadziwa.

3

1 Koma Mose analikuweta gulu la Yetero mpongozi wace, wansembe wa ku Midyani; natsogolera gululo m'tsogolo mwa cipululu, nafika ku phiri la Mulungu, ku Horebe.

2 Ndipo mthenga wa Molungu anamuonekera m'cirangali camoto coturuka m'kati mwa citsamba; ndipo anapenya, ndipo taonani, citsamba cirikuyaka moto, koma cosanyeka citsambaco.

3 Ndipo Mose anati, Ndipatuketu, ndikaone cooneka cacikuruco, citsambaco sicinyeka bwanji,

4 Pamene Yehova anaona kuti adapatuka kukapenya, Mulungu ali m'kati mwa citsamba, anamuitana, nati, Mose, Mose. Ndipo anati, Ndiri pano.

5 Ndipo iye anati, Usayandikire kuno; bvula nsapato zako ku mapazi ako, pakuti pamalo pamene upondapo iwe, mpopatulika.

6 Ananenanso Ine ndine Mulungu wa atate wako, Molungu wa Abrahamu, Molungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo. Ndipo Mose anabisa nkhope yace; popeza anaopa kuyang'ana Mulungu,

7 Ndipo Yehova anati, Ndapenyetsetsa mazunzo a anthu anga ali m'Aigupto, ndamvanso kulira kwao cifukwa ca akuwafulumiza; pakuti ndidziwa zowawitsa zao;

8 ndipo ndatsikira kuwalanditsa m'manja a anthu a Aigupto, ndi kuwatumtsa m'dziko lila akwere nalowe m'dziko labwino ndi lalikuru, m'dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi; ku malo a Akanani, ndi Ahiti ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi.

9 Ndipo tsopano, taona kulira kwa ana a Israyeli kwandifikira; ndapenyanso kupsinjika kumene Aaigupto awapsinja nako.

10 Tiye tsopano, ndikutuma kwa Farao, kuti uturutse anthu anga, ana a Israyeli m'Aigupto.

11 Koma Mose anati kwa Mulungu, Ndine yani ine kuti ndipite kwa Farao, ndi kuti nditurutse ana a Israyeli m'Aigupto?

12 Ndipo iye anati, Ine ndidzakhala ndi iwe; ndipo ici ndi cizindikilo ca iwe, cakuti ndakutuma ndine; utaturutsa anthuwo m'Aigupto mudzatumikira Mulungu paphiri pano.

13 Ndipo Mose anati kwa Mulungu, Onani, pakufika ine kwa ana a Israyeli, ndi kunena nao, Mulungu wa makolo anu wandituma kwa inu; ndipo akakanena ndi ine, Dzina lace ndani? ndikanena nao ciani?

14 Ndipo Molungu anati kwa Mose, INE NDINE YEMWE NDIRI INE. Anatinso, Ukatero ndi ana a Israyeli, INE NDINE wandituma kwa inu.

15 Ndipo Mulungu ananenanso kwa Mose, Ukatero ndi ana a Israyeli, Yehova, Molungu wa makolo anu, Molungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Molungu wa Yakobo anandituma kwa inu; ili nw dzina langa nthawi yosatha, ici ndi cikumbukiro canga m'mibadwo mibadwo.

16 Muka, nukasonkhanitse akuru a Israyeli, nunene nao, Yehova, Mulungu wa makolo anu anandionekera ine, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, ndi kuti; Ndakuzondani ndithu, ndi kuona comwe akucitirani m'Aigupto;

17 ndipo ndanena, Ndidzakukwezani kukuturutsani m'mazunzo a Aigupto, kukulowezani m'dziko la Akanani, ndi Ahiti, ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi, m'dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi.

18 Ndipo adzamveca mau ako; ndipo ukapite iwe ndi akuru a Israyeli, kwa mfumu ya Aigupto, ndi kukanena naye, Yehova, Mulungu wa Ahebri wakomana ndi ife; tiloleni, timuke tsopano ulendo wa masiku atatu m'cipululu, kuti timphere nsembe Yehova Mulungu wathu.

19 Koma Ine ndidziwa kuti mfumu ya Aigupto siidzalola inu kumuka, inde lingakhale ndi dzanja lamphamvu ai.

20 Ndipo ndidzatambasula dzanja langa, ndi kukantha Aigupto ndi zozizwa zanga zonse ndizicita pakati pace; ndi pambuyo pace adzakulolani kumuka.

21 Ndipo ndidzapatsa anthu awa ufulu pamaso pa anthu a Aigupto; ndipo kudzakhala, pamene muturuka simudzaturuka opanda kanthu;

22 koma mkazi yense adzafunse mnzace, ndi mlendo wokhala m'nyumba mwace, ampatse zokometsera zasiliva, ndi zokometsera zagolidi, ndi zobvala; ndipo mudzabveke nazo ana anu amuna ndi akazi; ndipo mudzafunkhe za Aaigupto.

4

1 Ndipo Mose anayankha nati, Koma taonani, sadzakhulupirira ine, kapena kumvera mau anga; pakuti adzanena, Yehova sanakuonekera iwe.

2 Ndipo Yehova ananena naye, Ico nciani m'dzanja lako? Nati, Ndodo.

3 Ndipo ananena iye, Iponye pansi. Naiponya pansi, ndipo inasanduka njoka; ndipo Mose anaithawa.

4 Koma Yehova anati kwa Mose, Tambasula dzanja lako, nuigwire kumcira; ndipo anatambasula dzanja lace, naigwira, nikhalanso ndodo m'dzanja lace;

5 kuti akhulupirire kuti wakuonekera Yehova Mulungu wa makolo ao, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.

6 Ndipo Yehova ananenanso naye, Longa dzanja lako pacifuwa pako. Ndipo analonga dzanja lace pacifuwa pace, naliturutsa, taonani, dzanja lace linali lakhate, lotuwa ngati cipale cofewa.

7 Ndipo ananena iye, Bwerezanso dzanja lako pacifuwa pako. Ndipo anabwerezanso dzanja lace pacifuwa pace; naliturutsa pacifuwa pace, taonani, linasandukanso lomwe lakale.

8 Ndipo kudzatero, ngati sakhulupirira iwe, ndi kusamvera mau a cizindikilo coyamba, adzakhulupirira mau a cizindikilo cotsirizaci.

9 Ndipo kudzatero, aka panda kukhulupirira zingakhale zizindikilo izi, ndi kusamvera mau ako, ukatunge madzi a kunyanja, ndi kuthira pamtunda; ndi madzi watunga ku nyanjayo adzasanduka mwazi pamtunda.

10 Ndipo Mose anati kwa Yehova, Mverani, Ambuye, ine ndine munthu wosowa ponena, kapena dzulo, kapena kale, kapena cilankhulire Inu ndi kapolo wanu, pakuti ndine wa m'kamwa molemera, ndi wa lilime lolemera.

11 Koma Yehova ananena naye, Anampangira munthu m'kamwa ndani? Kapena analenga munthu wosalankhula ndani, kapena wogontha, kapena wamaso, kapena wakhungu? Si ndine Yehova kodi?

12 Ndipo tsopano muka, ndipo Ine ndidzakhala m'kamwa mwako, ndi kukuphunzitsa comwe ukalankhule.

13 Koma anati, Mverani, Ambuye, tumizani pa dzanja la iye amene mudzamtuma.

14 Pamenepo mkwiyo wa Yehova unamyakira Mose, ndipo anati, Nanga Aroni Mlevi mbale wako sialipo kodi? Ndidziwa kuti kulankhula alankhula. Ndipo, taona, aturuka kudzakomana ndiwe; ndipo pakuona iwe adzakondweram'mtima mwace.

15 Ndipo ukalankhule naye, ndi kumpangira mau; ndipo Ine ndidzakhala m'kamwa mwako, ndi m'kamwa mwace, ndipo ndidzakuphunzitsani inu cimene mukacite.

16 Ndipo iye adzakulankhulira iwe kwa anthu; ndipo kudzatero, kuti iye adzakhala kwa iwe ngati m'kamwa, ndi iwe udzakhala kwa iye ngati Mulungu.

17 Ndipo ukaigwire m'dzanja lako ndodo iyi, imene ukacite nayo zizindikilozo.

18 Ndipo Mose anabwera namuka kwa Yetero mpongozi wace, nanena naye, Ndimuketu, ndibwerere kumka kwa abale anga amene ali m'Aigupto, ndikaone ngati akali ndi moyo. Ndipo Yetero ananena ndi Mose, Pita bwino.

19 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'Midyani, Muka, bwerera kumka ku Aigupto; pakuti adafa anthu onse amene anafuna moyo wako.

20 Pamenepo Mose anatenga mkazi wace ndi ana ace amuna, nawakweza pa buru, nabwerera kumka ku dziko la Aigupto; ndipo Mose anagwira ndodo ya Mulungu m'dzanja lace.

21 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Pakumuka iwe kubwerera kumka ku Aigupto, usamalire ucite zozizwa zonse ndaziika m'dzanja lako, pamaso pa Farao; koma Ine ndidzalimbitsa mtima wace kuti asadzalole anthu kupita.

22 Pamenepo ukanene ndi Farao, Atero Yehova, Mwana wanga, mwana wanga woyamba ndiye Israyeli.

23 Ndipo ndanena ndi iwe, Mlole mwana wanga amuke, kuti anditumikire Ine; koma wakana kumlola kuti asamuke; taona, Ine ndidzamupha mwana wako wamwamuna, mwana wako woyamba.

24 Ndipo kunali panjira, kucigono, Yehova anakomana naye, nafuna kumupha.

25 Koma Zipora anatenga mpeni wamwala, nadula khungu la mwana wace, naliponya pa mapazi ace; nati, Pakuti iwe ndiwe mkwati wanga wamwazi. Ndipo iye anamleka.

26 Pamenepo anati mkaziyo, Mkwati wamwazi iwe, cifukwa ca mdulidwe.

27 Ndipo Yehova ananena ndi Aroni, Muka kucipululu kukakomana ndi Mose. Ndipo anamuka, nakomana naye pa phiri la Mulungu, nampsompsona.

28 Ndipo Mose anauza Aroni mau onse a Yehova amene adamtuma nao, ndi zizindikilo zonse zimene adamlamulira.

29 Pamenepo Mose ndi Aroni anamuka nasonkhanitsa akuru onse a ana a Israyeli;

30 ndipo Aroni anawafotokozera mau onse amene Yehova adauza Mose, nacita zizindikilo zija pamaso pa anthu.

31 Ndipo anthuwo anakhulupirira; ndipo pamene anamva kuti Yehova adawazonda ana a Israyeli, ndi kuti adaona mazunzo ao, anawerama, nalambira Mulungu.

5

1 Ndipo pambuyo pace Mose ndi Aroni analowa nanena ndi Farao, Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli, Lola anthu anga apite, kundicitira madyerero m'cipululu.

2 Koma Farao anati, Yehova ndani, kuti ndimvere mau ace ndi kulola Israyeli apite? Sindimdziwa Yehova, ndiponso sindidzalola Israyeli apite.

3 Ndipo iwo anati, Mulungu wa Ahebri wakomana ndi ife; timuketu ulendo wa masiku atatu m'cipululu, kumphera nsembe Yehova Mulungu wathu; kuti angatikumike ndi mliri, kapena ndi lupanga,

4 Ndipo mfumu ya Aigupto inanena nao, Inu, Mose ndi Aroni, cifukwa ninji mumasulira anthu nchito zao? Mukani ku akatundu anu.

5 Farao anatinso, Taonani, anthu a m'dziko ndiwo ambiri tsopano; ndipo inu muwapumitsa ku akatundu ao,

6 Ndipo tsiku lomwelo Farao analamulira akufulumiza anthu, ndi akapitao ao, ndi kuti,

7 Musawapatsanso anthu udzu wakupanga nao njerwa monga kale; apite okha adzifunire udzu.

8 Ndipo muziwawerengera njerwa, monga momwe anapanga kale; musacepsapo, popeza acita cilezi; cifukwa cace alikupfuula, ndi kuti, Timuke, timphere nsembe Mulungu wathu.

9 Ilimbike nchito pa amunawo, kuti aigwiritsitse, asasamalire mau amabodza.

10 Ndipo akufulumiza anthu ndi akapitao ao anaturuka, nanena ndi anthu ndi kuti, Atero Farao, Kulibe kukupatsani udzu.

11 Mukani inu nokha, dzifunireni udzu komwe muupeza; pakuti palibe kanthu kadzacepa pa nchito yanu.

12 Pamenepo anthuwo anabalalika m'dziko lonse la Aigupto kufuna ciputu ngati udzu.

13 Ndipo akufulumiza anawakakamiza, ndi kuti, Tsirizani nchito zanu, nchito ya tsiku pa tsiku lace, monga muja munali ndi udzu.

14 Ndipo anapanda akapitao a ana a Israyeli, amene ofulumiza a Farao adawaika, ndi kuti, Nanga dzulo ndi lero simunatsiriza bwanji nchito yanu yoneneka ya njerwa, monga kale?

15 Pamenepo akapitao a ana a Israyeli anafika nalirira Farao, nati, Mwatero bwanji ndi akapolo anu?

16 Udzu osawapatsa akapolo anu, ndipo amanena ndi ife, Umbani njerwa; ndipo, taonani, amapanda akapolo anu; koma kulakwa nkwa anthu anu.

17 Koma iye anati, Aulesi inu, aulesi: cifukwa cace mulikunena, Timuke, timphere nsembe Yehova.

18 Mukani tsopano, gwirani nchito; pakuti sadzakupatsani udzu, koma muonetse ciwerengero cace ca njerwa.

19 Ndipo akapitao a ana a Israyeli anaona kuti kudawaipira, pamene ananena, Musamacepetsa njerwa zanu, nchito ya tsiku pa tsiku lace.

20 Ndipo poturuka kwa Farao iwo anakomana ndi Mose ndi Aroni, alikuima popenyana nao;

21 ndipo ananena nao, Yehova akupenyeni, naweruze; pakuti mwatinyansitsa pamaso pa Farao, ndi pamaso pa anyamata ace, ndi kuwapatsa lupanga m'dzanja lao kutipha nalo.

22 Pamenepo Mose anabwerera namka kwa Yehova, nati, Ambuye, mwawacitiranji coipa anthuwa? mwandituma bwanji?

23 Popeza kuyambira kuja ndinafika kwa Farao kulankhula m'dzina lanu, anawacitira coipa anthuwa; ndipo simunalanditsa anthu anu konse.

6

1 Ndipo Yehova ananena kwa Mose, Tsopano udzaona comwe ndidzacitira Farao; pakuti ndi dzanja lamphamvu adzawalola apite, inde ndi dzanja lamphamvu adzawaingitsa m'dziko lace.

2 Ndipo Mulungu ananena ndi Mose, nati kwa iye, Ine ndine YEHOV A:

3 ndipo ndinaonekera Abrahamu, Isake ndi Yakobo, Mulungu Wamphamvuyonse; koma sindinadziwika kwa iwo ndi dzina langa YEHOV A.

4 Ndipo ndinakhazikitsanso nao cipangano canga, kuwapatsa dziko la Kanani, dziko la maulendo ao, anali alendo m'mwemo.

5 Ndamvanso kubuula kwa ana a Israyeli, amene Aaigupto awayesa akapolo; ndipo ndakumbukila cipangano canga.

6 Cifukwa cace nena kwa ana a Israyeli, Ine ndine Yehova, ndipo ndidzakuturutsani pansi pa akatundu a Aaigupto, ndipo ndidzakulanditsani ku ukapolo wanu; ndipo ndidzakuombolani ndi dzanja lotambasuka, ndi maweruzo akuru;

7 ndipo ndidzalandira inu mukhale anthu anga, ndipo ndidzakhala Ine Mulungu wanu; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, wakuturutsa inu pansi pa akatundu a Aaigupto.

8 Ndipo ndidzakulowetsani m'dziko limene ndinakweza dzanja langa kunena za ilo, kuti ndilipereke kwa Abrahamu, kwa Isake ndi kwa Yakobo; ndipo ndidzakupatsani ilo likhale lanulanu; Ine ndine Yehova.

9 Ndipo Mose ananena comweco ndi ana a Israyeli; koma sanamvera Mose cifukwa ca kuwawa mtima, ndi ukapolo wolemera.

10 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

11 Lowa, lankhula ndi Farao mfumu ya Aigupto, kuti alole ana a Israyeli aturuke m'dziko lace.

12 Koma Mose ananena pamaso pa Mulungu, ndi kuti, Onani, ana a Israyeli sanandimvera ine; adzandimvera bwanji Farao, ndine wa milomo yosadula?

13 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nawalangiza za ana a Israyeli, ndi za Farao mfumu ya Aigupto, kuti aturutse ana a Israyeli m'dziko la Aigupto.

14 Akuru a mbumba za makolo ao ndi awa: ana amuna a Rubeni, woyamba wa Israyeli ndiwo: Hanoki ndi Palu, Hezroni, ndi Karmi; amene ndiwo mabanja a Rubeni.

15 Ndi ana amuna a Simeoni ndiwo: Yemweli, ndi Yamini, ndi Ohadi, Yakini, ndi Zohari, ndi Sauli mwana wa mkazi wa m'Kanani; amene ndiwo mabanja a Simeoni.

16 Ndipo maina a ana amuna a Levi, mwa kubadwa kwao ndiwo: Gerisoni, ndi Kohati, ndi Merari; ndipo zaka za moyo wa Levi ndizo zana limodzi mphambu makumi atatu kudza zisanu ndi ziwiri.

17 Ana amuna a Gerisoni ndiwo: Libni ndi Simei, mwa mabanja ao.

18 Ndi ana amuna a Kohati ndiwo: Amramu ndi Izara, ndi Hebroni, ndi Uziyeli; ndipo zaka za moyo wa Kohati ndizo zana limodzi ndi makumi atatu kudza zitatu.

19 Ndipo ana amuna a Merai ndiwo: Mali ndi Musi. Amenewo ndiwo mabanja a Levi mwa kubadwa kwao.

20 Ndipo Amramu anadzitengera Yokobedi mlongo wa atate wace akhale mkazi wace; ndipo anambalira Aroni ndi Mose; ndi zaka za moyo wa Amramu ndizo zaria limodzi mphambu makumi atatu kudza zisanu ndi ziwiri.

21 Ndi ana amuna a lzara ndiwo: Kora: ndi Nefegi, ndi Zikiri.

22 Ndi ana amuna a Uziyeli ndiwo: Misayeli, ndi Elisafana, ndi Sitiri.

23 Ndipo Aroni anadzitengera Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wace wa Nasoni, akhale mkazi wace; ndipo anambalira Nadabu ndi Abihu, Eleazara ndi ltamara.

24 Ndipo ana amuna a Kora ndiwo: Asiri ndi Elikana, ndi Abiasafu; amenewo ndiwo mabanja a Akora.

25 Ndipo Eleazara mwana wa Aroni anadzitengera mkazi wa ana akazi a Putieli akhale mkazi wace, ndipo anambalira Pinehasi. Amenewo ndi akuru a makolo a Alevi mwa mabanja ao.

26 Omwewo ndiwo Aroni ndi Mose amene Yehova ananena nao, Turutsani ana a Israyeli m'dziko la Aigupto mwa makamu ao.

27 Awa ndi omwewo ananena ndi Farao, mfumu ya Aigupto, awaturutse ana a Israyeli m'Aigupto; Mose ndi Aroni amenewa.

28 Ndipo kunali, tsiku limene Yehova ananena ndi Mose m'dziko la Aigupto,

29 Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti, Ine ndine Yehova: lankhula ndi Farao mfumu ya Aigupto zonsezi Ine ndizinena nawe.

30 Koma Mose anati pamaso pa Yehova, Onani, ine ndiri wa milome yosadula, ndipo Farao adzandimvera bwanji?

7

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Taona, ndakuika ngati Mulungu kwa Farao; ndi Aroni mkuru wako adzakhala mneneri wako.

2 Iwe uzdankhula zonse ndikulamulira; ndi Aroni mkuru wako azilankhula kwa Farao, kuti alole ana a Israyeli aturuke m'dziko lace.

3 Koma Ine ndidzaumitsa mtima wace wa Farao, ndipo ndidzacurukitsa zizindikilo ndi zozizwa zanga m'dziko la Aigupto.

4 Koma Farao sadzamvera inu, ndipo ndidzaika dzanja langa pa Aigupto, ndipo ndidzaturutsa makamu anga, anthu anga ana a Israyeli, m'dziko la Aigupto ndi maweruzo akuru.

5 Ndipo Aaigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pakutambasula Ine dzanja langa pa Aigupto, ndi kuturutsa ana a Israyeli pakati pao.

6 Ndipo Mose ndi Aroni anacita monga Yehova anawalamulira, momwemo anacita.

7 Ndipo Mose anali nazo zaka makumi asanu ndi atatu, ndi Aroni anali nazo zaka makumi asanu ndi atatu kudza zitatu, pamene ananena ndi Farao.

8 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, ndi kuti,

9 Pamene Farao adzalankhula nanu, ndi kuti, Dzicitireni codabwiza; pamenepo uzinena ndi Aroni, Tenga ndodo yako, Iponye pansi pamaso pa Farao, isanduke cinjoka,

10 Ndipo Mose ndi Aroni analowa kwa Farao, nacita monga momwe Yehova adawalamulira; ndipo Aroni anaponya pansi ndodo yace pamaso pa Farao, ndi pamaso pa anyamata ace, ndipo inasanduka cinjoka,

11 Pamenepo Farao anaitananso anzeru, ndi amatsenga; ndipo alembi a Aigupto, iwonso anacita momwemo ndi matsenga ao.

12 Pakuti yense anaponya pansi ndodo yace, ndipo zinasanduka zinjoka; koma ndodoya Aroni inameza ndodo zao,

13 Koma mtima wa Farao unalimba, ndipo sanamvera iwo; monga adalankhula Yehova.

14 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Walemera mtima wa Farao, akana kulola anthu apite,

15 Muka kwa Farao m'mawa; taona, aturuka kumka kumadzi; nuime kumlinda m'mbali mwa nyanja; ndi ndodo idasanduka njokayo uigwire m'dzanja lako.

16 Ndipo ukanena naye, Yehova, Mulungu wa Ahebri anandituma kwa inu, ndi kuti, Lola anthu anga amuke kuti anditumukire m'cipululu; koma, taona, sunamvera ndi pano.

17 Atero Yehova, Ndi ici udzadziwa kuti Ine ndine Yehova: taonani, ndidzapanda madzi ali m'nyanja ndi ndodo iri m'dzanja langa, ndipo adzasanduka mwazi.

18 Ndi nsomba ziri m'nyanja zidzafa, ndi nyanja idzanunkha; ndi Aaigupto adzacita mtima useru ndi kumwa madzi a m'nyanjamo.

19 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Nena ndi Aroni, Tenga ndodo yako, nutambasule dzanja lako pa madzi a m'Aigupto, pa nyanja yao, pa ngalande zao, ndi pa matamanda ao, ndi pa matawale ao onse amadzi, kuti asanduke mwazi; mukhale mwazi m'dziko lonse la Aigupto, m'zotengera zamtengo, ndi zamwala.

20 Ndipo Mose ndi Aroni anacita monga momwe Yehova adawalamulira; nasamula ndodo, napanda madzi ali m'nyanjamo pamaso pa Farao, ndi pamaso pa anyamata ace; ndipo madzi onse a m'nyanjamo anasanduka mwazi.

21 Ndi nsomba za m'nyanjamo zinafa; ndi nyanjayo inanunkha; ndipo Aaigupto sanakhoza kumwa madzi a m'nyanjamo; ndipo munali mwazi m'dziko lonse la Aigupto.

22 Ndipo alembi a Aigupto anacita momwemo ndi matsenga ao; koma mtima wa Farao unalimba, ndipo sanamvera iwo; monga adalankhula Yehova.

23 Ndipo Farao anatembenuka, nalowa m'nyumba yace, osasamalira ici comwe mumtima mwace.

24 Koma Aaigupto onse anakumba m'mphepete mwa nyanja kufuna madzi akumwa; pakuti sanakhoza kumwa madzi a m'nyanjamo.

25 Ndipo anafikiramasiku asanu ndi awiri atapanda nyanja Yehova.

8

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Lowa kwa Farao, nunene naye, Atero Yehova, Lola anthu anga amuke, kuti anditumikire.

2 Ndipo ukakana kuwalola amuke, taona, Ine ndidzapanda dziko lako lonse ndi acule;

3 ndipo m'nyanjamo mudzacuruka acule, amene adzakwera nadzalowa m'nyumba mwako, ndi m'cipinda cogona iwe, ndi pakama pako, ndi m'nyumba ya anyamata ako, ndi pa anthu ako, m'micembo yanu yooceramo, ndi m'mbale zanu zoumbiramo.

4 Ndipo acule adzakwera pa iwe, ndi pa anthu ako, ndi pa anyamata ako onse.

5 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Nena ndi Aroni, Tambasula dzanja lako ndi ndodo yako, panyanja, pangalande, ndi pamatamanda, nukweretse acule pa dziko la Aigupto.

6 Ndipo Aroni anatambasula dzanja lace pa madzi a m'Aigupto; ndipo anakwera acule, nakuta dziko la Aigupto.

7 Ndipo alembi anacita momwemo ndi matsenga ao, nakweretsa acule pa dziko la Aigupto.

8 Pamenepo Farao anaitana Mose ndi Aroni, nati, Mundipembere Yehova, kuti andicotsere ine ndi anthu anga aculewo; ndipo ndidzalola anthu amuke, kuti amphere Yehova nsembe.

9 Koma Mose anati kwa Farao, Ulemu ndi wanu, wa ine ai; ndipembere inu ndi anyamata anu ndi anthu anu liti, kuti aonongeke aculewo, acokere inu ndi nyumba zanu, atsale m'nyanja mokha?

10 Ndipo anati, Mawa. Nati Mose, Kukhale monga mau anu, kuti mudziwe, kuti palibe wina wonga Yehova Mulungu wathu.

11 Ndipo acule adzacokera inu, ndi nyumba zanu, ndi anyamata anu, ndi anthu anu; adzatsala m'nyanja mokha.

12 Ndipo Mose ndi Aroni anaturuka kwa Farao; ndi Mose anapfuulira kwa Yehova kunena za acule amene adawaika pa Farao.

13 Ndipo Yehova anacita monga mwa mau a Mose; nafa aculewo kucokera m'zinyumba, ndi m'mabwalo, ndi m'minda.

14 Ndipo anawaola miulu-miulu; ndi dziko linanunkha.

15 Koma pamene Farao, anaona kuti panali kupuma, anaumitsa mtima wace, osamvera iwo; monga adalankhula Yehova.

16 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Nena ndi Aroni, Samula ndodo yako, nupande pfumbi lapansi, kuti lisanduke nsabwe m'dziko lonse la Aigupto.

17 Ndipo anacita comweco; pakuti Aroni anasamula dzanja lace ndi ndodo yace, napanda pfumbi lapansi, ndipo panali nsabwe pa anthu ndi pa zoweta; pfumbi lonse lapansi liinasanduka nsabwe m'dziko lonse la Aigupto.

18 Alembi anateronso ndi matsenga ao kuonetsa nsabwe, koma sanakhoza; ndipo panali nsabwe pa anthu, ndi pa zoweta.

19 Pamenepo alembi anati kwa Farao, Cala ca Mulungu ici; koma mtima wa Farao unalimba, osamvera iwo; monga adalankhula Yehova.

20 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Uuke ulawire mamawa, nuime pamaso pa Farao; taona, aturuka kumka kumadzi; nunene naye, Atero Yehova, Lola anthu anga amuke, anditumikire.

21 Pakuti ukapanda kulola anthu anga amuke, taona, ndidzatuma mizaza pa iwe, ndi pa anyamata ako, ndi pa anthu ako, ndi pa nyumba zako; ndipo nyumba za Aaigupto zidzadzala nayo mizaza, ndi nthaka yomwe imene ikhalapo.

22 Ndipo tsiku ilo ndidzalemba malire dziko la Goseni, m'mene mukhala anthu anga, kuti pamenepo pasakhale mizaza; kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova pakati pa dzikoli.

23 Ndipo ndidzaika cosiyanitsa pakati pa anthu anga ndi anthu ako; mawa padzakhala cizindikilo ici.

24 Ndipo Yehovaanacita comweco; ndipo kunafika magulu a mizaza m'nyumba ya Farao, ndi m'nyumba za anyamata ace, ndi m'dziko lonse la Aigupto; dziko linaipatu cifukwa ca mizazayo.

25 Pamenepo Farao anaitana Mose ndi Aroni, nati, Mukani, mphereni nsembe Mulungu wanu m'dzikomu.

26 Koma Mose anati, Sikuyenera kutero; pakuti tidzamphera Yehova Mulungu wathu conyansa ca Aaigupto; taonani, ngati tikamphera nsembeconyansaca Aaigupto pamaso pao sadzatiponya miyala kodi?

27 Timuke ulendo wa masiku atatu m'cipululu, tikamphere Yehova Mulungu wathu nsembe, monga adzanena nafe.

28 Ndipo Farao anati, Ndidzakulolani mumuke, kuti mukamphere nsembe Yehova. Mulungu wanu m'cipululu; komatu musamuke kutaritu: mundipembere.

29 Ndipo Mose anati, Onani, ndirikuturuka ine kwanu, ndidzapemba Yehova kuti mizaza icoke mawa kwa Farao, ndi kwa anyamata ace, ndi kwa anthu ace; komatu, Farao asanyengenso ndi kukana kulola anthuwa amuke kukamphera nsembe Yehova.

30 Ndipo Mose anaturuka kwa Farao, napemba Yehova.

31 Ndipo Yehova anacita monga mwa mau a Mose; nacotsera Farao ndi anyamata ace ndi anthu ace mizazayo, sunatsala ndi umodzi wonse.

32 Koma Farao anaumitsa mtima wace nthawi yomweyonso, ndipo sanalola anthu amuke.

9

1 Pamenepo Yehova anati kwa Mose, Lowa kwa Farao, numuuze, Atero Yehova Mulungu wa Ahebri, Lola anthu anga amuke, kuti anditumikire.

2 Pakuti ukakana kuwalola amuke, ndi kuwagwira cigwiritsire,

3 taona, dzanja la Yehova lidzakhala pa zoweta zako za kubusa, pa akavalo, pa aburu, pa ngamila, pa ng'ombe, ndi pa zoweta zazing'ono ndi kalira woopsa.

4 Ndipo Yehova adzasiyanitsa pakati pa zoweta za Israyeli ndi zoweta za Aigupto; kuti kasafe kanthu kali konse ka ana a Israyeli,

5 Ndipo Yehova anaika nthawi yakuti, nati, Mawa Yehova adzacita cinthu ice m'dzikomu.

6 Ndipo m'mawa mwace Yehova anacita cinthuco, ndipo zinafa zoweta zonse za m'Aigupto; koma sicinafa cimodzi conse ca zoweta za ana a Israyeli.

7 Ndipo Farao anatuma, taonani, sicidafa cingakhale cimodzi comwe ca zoweta za Aisrayeli. Koma mtima wa Farao unauma, ndipo sanalola anthu amuke.

8 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, Tengani phulusa la ng'anjo lodzala manja; ndi Mose aliwaze kuthambo pamaso pa Farao.

9 Ndipo lidzakhala pfumbi losalala pa dziko lonse la Aigupto, ndipo lidzakhala pa anthu ndi pa zoweta ngati zironda zobuka ndi matuza, m'dziko lonse la Aigupto.

10 Ndipo anatenga phulusa la m'ng'anjo, naima pamaso pa Farao; ndi Mose analiwaza kuthambo; ndipo linakhala zironda zobuka ndi matuza pa anthu ndi pa zoweta.

11 Ndipo alembi sanakhoza kuima pamaso pa Mose cifukwa ca zirondaw; popeza panali zironda pa alembi ndi pa Aaigupto onse.

12 Koma Yehova analimbitsa mtima wa Farao, kuti sanamvera iwo; moga Yehova adalankhula ndi Mose.

13 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Uka oulawire mamawa, nuime pamaso pa Farao, nunene naye, Atero Yehova, Mulungu wa Ahebri, Lola anthu anga amuke, akanditumikire.

14 Pakuti nthawi yino ndidzatuma miliri yanga yonse pamtima pako, ndi pa anayamata ako, ndi pa anthu ako; kuti udziwe kuti palibe wina wonga Ine pa dziko lonse lapansi.

15 Pakuti ndatambasula dzanja langa tsopano, kuti ndikupande iwe ndi anthu ako ndi mliri, ndi kuti uonoogeke pa dziko lapansi.

16 Koma ndithu cifukwa cace ndakuimika kuti ndikuonetse mphamvu yanga, ndi kuti alalikire dzina langa pa dziko lonse lapansi.

17 Kodi udzikwezanso pa anthu anga, ndi kusawalola amuke?

18 Taona, mawa monga nthawi yino ndidzabvumbitsa mbvumbi wa matalala, sipadakhala unzace m'Aigupto kuyambira tsiku lija lidakhazikika kufikira lero lino.

19 Ndipo tsopano, tumiza, thawitsa zoweta zako ndi zonse uli nazo pabwalo; pakuti anthu onse ndi zoweta zonse zopezeka pabwalo, zosasonkhanidwa m'nyumba, matalala adzazigwera, ndipo zidzafa.

20 Iyeyu wa anyamata a Farao wakuopa mau a Yehova anathawitsira m'zinyumba anyamata ace ndi zoweta zace;

21 koma iyeyu wosasamalira mau a Yehova anasiya anyamata ndi zoweta zace kubusa.

22 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tambasula dzanja lako kuthambo, kuti pakhale matalala pa dziko lonse la Aigupto, pa anthu ndi pa zoweta, ndi pa zitsamba zonse za kuthengo, m'dziko la Aigupto.

23 Pamenepo Mose anasamulira ndodo yace kuthambo, ndipo Yehova anatumiza bingu ndi matalala, ndi moto unatsikira pansi; ndipo Yehova anabvumbitsa matalala pa dziko la Aigupto.

24 Potero panali matalala, ndi mota wakutsikatsika pakati pa matalala, coopsa ndithu; panalibe cotere m'dziko lonse la Aigupto ciyambire mtundu wao.

25 Ndipo matalala anapanda m'dziko lonse la Aigupto zonse za pabwalo, kuyambira anthu kufikira zoweta; ndipo matalala anapanda zitsamba zonse za kuthengo, nathyola mitengo yonse ya kuthengo.

26 M'dziko la Goseni mokha, mokhala ana a Israyeli, munalibe matalala.

27 Ndipo Farao anatumiza, naitana Mose ndi Aroni, nanena nao, Ndacimwa tsopano; Yehova ndiye wolungama, ine ndi anthu anga ndife oipa,

28 Pembani kwa Yehova; cifukwa akwanira ndithu mabingu a Mulungu ndi matalala; ndipo ndidzakulolani mumuke, osakhalanso.

29 Ndipo Mose ananena naye, Poturuka m'mudzi ine, ndidzasasatulira manja anga kwa Yehova; mabingu adzaleka, ndi matalala sadzakhalaponso; kuti mudziwe kuti dziko lapansi nla Yehova.

30 Koma inu ndi anyamata anu ndidziwa kuti simudzayamba kuopa nkhope ya Yehova Mulungu.

31 Ndipo thonje ndi barele zinayoyoka; pakuti barele lidafura, ndi thonje lidayamba maluwa.

32 Koma tirigu ndi rai sizinayoyoka popeza amabzala m'mbuyo.

33 Ndipo Mose anaturuka kwa Farao m'mudzi nasasatulira manja ace kwa Yehova; ndipo mabingu ndi matalala analeka, ndi mvula siinabvumbanso padziko.

34 Pamene Farao anaona kuti mvula ndi matalala ndi mabingu zidaleka anaonjezanso kucimwa, naumitsa mtima wace, iye ndi anyamata ace.

35 Potero mtima wa Farao unalimba, ndipo sanalola ana a Israyeli amuke; monga Yehova adalankhula mwa Mose.

10

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Lowa kwa Farao; pakuti ndaumitsa mtima wace, ndi mtima wa anyamata ace, kuti ndiike zizindikilo zanga izi pakati pao;

2 ndi kuti ufotokozere, m'makutu a ana ako, ndi a zidzukulu zako, comwe ndidzacita m'Aigupto, ndi zizindikilo zanga zimene ndinaziika pakati pao; kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova.

3 Ndipo Mose ndi Aroni analowa kwa Farao nanena naye, Atero Yehova, Mulungu wa Ahebri, Ukana kudzicepetsa pamaso panga kufikira liti? Lola anthu anga amuke, akanditumikire;

4 pakuti ukakana kulola anthu anga amuke, taona, mawa ndidzafikitsa dzombe m'dziko lako;

5 ndipo lidzakuta nkhope ya dziko, kotero, kuti palibe munthu adzakhoza kuona dziko; ndipo lidzadya zotsalira zidapulumuka, zidatsalira inu pamatalala, ndipo lidzadya mtengo uti wonse wokuphukirani kuthengo;

6 ndipo lidzadzaza m'nyumba zako, ndi m'nyumba za anyamata ako onse, ndi m'nyumba za Aaigupto onse; sanaciona cotere atate ako kapena makolo ako, kuyambira tsiku lija lakukhala iwo pa dziko lapansi kufikira lero lino. Ndipo anatembenuka, naturuka kwa Farao.

7 Ndipo anyamata ace a Farao ananena naye, Ameneyo amaticitira msampha kufikira liti? Lolani anthuwo amuke, akatumikire Yehova Mulungu wao. Kodi simunayambe kudziwa kuti Aigupto laonongeka?

8 Ndipo anawabwereretsa Mose ndi Aroni kwa Farao, nanena nao, Mukani, katumikireni Yehova Mulungu wanu. Koma amene adzapitawo ndiwo ani?

9 Ndipo Mose anati, Tidzamuka ndi ana athu ndi akuru athu, ndi ana athu amuna ndi akazi; tidzamuka nazo nkhosa zathu ndi ng'ombe zathu; pakuti tiri nao madyerero a Yehova.

10 Ndipo ananena nao, Momwemo, Yehova akhale nanu ngati ndilola inu ndi ana ang'ono anu mumuke; cenjerani, pakuti pali coipa pamaso panu,

11 Cotero ai, mukani tsopano, inu amuna akuru, tumikirani Yehova pakuti ici mucifuna. Ndipo anawapitikitsa pamaso pa Farao.

12 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tambasulira dzanja lako pa dziko la Aigupto, lidze dzombe, kuti likwere pa dziko la Aigupto, lidye zitsamba zonse za m'dziko, ndizo zonse adazisiya matalala.

13 Pamenepo Mose analoza ndodo yace pa dziko la Aigupto; ndipo Yehova anaombetsa padziko mphepo ya kum'mawa usana wonse, ndi usiku womwe; ndipo kutaca mphepo ya kum'mawa inadza nalo dzombe.

14 Ndipo dzombe linakwera pa dziko lonse la Aigupto, ndipo linatera pakati pa malire onse a Aigupto, lambirimbiri; lisanafike ili panalibe dzombe lotere longa ili, ndipo litapita ili sipadzakhalanso lotere.

15 Pakuti linakuta nkhope ya dziko lonse kuti dziko linada; ndipo linadya zitsamba zonse za m'dziko, ndi zipatso zonse za mitengo zimene matalala adazisiya; ndipo sipanatsala cabiriwiri ciri conse, pamitengo kapena pa zitsamba za kuthengo, m'dziko lonse la Aigupto.

16 Pamenepo Farao anafulumira kuitana Mose ndi Aroni; nati, Ndalakwira Yehova Mulungu wanu, ndi inu.

17 Ndipo tsopano, ndikhululukirenitu kulakwa kwanga nthawi yino yokha, nimundipembere kwa Yehova Mulungu wanu, kuti andicotsere imfa yino yokha.

18 Ndipo anaturuka kwa Farao, napemba Yehova.

19 Ndipo Yehova anabweza mphepo yolimbatu ya kumadzulo, imene inapita nalo dzombe niliponya m'Nyanja Yofiira: silinatsala dzombe limodzi pakati pa malire onse a Aigupto.

20 Koma Yehova analimbitsa mtima wa Farao, ndipo sanalola ana a Israyeli amuke.

21 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tambasulira dzanja lako kuthambo, ndipo padzakhala mdima pa dziko la Aigupto, ndiwo mdima wokhudzika.

22 Ndipo Mose anatambasulira dzanja lace kuthambo; ndipo munali mdima bii m'dziko lonse la Aigupto masiku atatu;

23 sanaonana, sanaukanso munthu pamalo pace, masiku atatu; koma kwa ana onse a Israyeli kudayera m'nyumba zao.

24 Ndipo Farao anaitana Mose, nati, Mukani, tumikirani Yehova; nkhosa zanu ndi ng'ombe zanu zokha zitsale; mumuke nao ana anu ang'ononso.

25 Koma Mose anati, Mutipatsenso m'dzanja mwathu nsembe zophera ndi nsembe zopsereza, kuti timkonzere Yehova Mulungu wathu.

26 Zoweta zathu zomwe tidzapita nazo; cosatsala ciboda cimodzi; pakuti mwa izo tiyenera kutenga zakutumikira nazo Yehova Mulungu wathu; ndipo tisanafikeko, sitidziwa umo tidzamtumikira Yehova.

27 Koma Yehova analimbitsa mtima wace wa Farao, ndipo anakana kuwaleka amuke.

28 Ndipo Farao ananena naye, Coka pano, uzicenjera usaonenso nkhope yanga; pakuti tsiku limene uonanso nkhope yanga udzafa.

29 Ndipo Mose anati, Mwanena bwino; sindidzaonanso nkhope yanu.

11

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Watsala moo umodzi ndidzamtengera Farao, ndi Aigupto; pambuyo pace adzakulolani mucoke kuno; pamene akulolani kupita, zoonadi adzakuingitsani kuno konse.

2 Lankhula tsopano m'makutu a anthu, kuti mwamuna yense apemphe kwa mnzace, ndi mkazi yense kwa mnzace, zokometsera zasiliva ndi zagolidi.

3 Ndipo Yehova anawapatsa anthu cisomo pamaso pa Aaigupto. Munthuyo Mose ndiyenso wamkuru ndithu m'dziko la Aigupto, pamaso pa anyamata a Farao, ndi pamaso pa anthu.

4 Ndipo Mose anati, Atero Yehova, Monga pakati pa usiku ndidzaturuka loe kumka pakati pa Aigupto;

5 ndipo ana onse oyamba a m'dziko la Aigupto adzafa, kuyambira mwana woyamba wa Farao wokhala pa mpando wacifumu wace, kufikira mwana woyamba wa mdzakazi wokhala pa miyala yopera; ndi ana onse oyamba a zoweta.

6 Ndipo kudzakhala kulira kwakukuru m'dziko lonse la Aigupto, kunalibe kunzace kotere, sikudzakhalanso kunzace kotere.

7 Koma palibe garu adzafunyitsira lilime lace ana onse a Israyeli ngakhale anthu kapena zoweta; kuti mudziwe kuti Yehova asiyanitsa pakati pa Aaigupto ndi Aisrayeli.

8 Ndipo anyamata ako onse awa adzanditsikira, nadzandigwadira, ndi kuti, Turukani inu, ndi anthu onse akukutsatani; ndipo pambuyo pace ndidzaturuka. Ndipo anaturuka kwa Farao wakupsa mtima.

9 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Farao sadzamvera inu; kuti zozizwa zanga zicuruke m'dziko la Aigupto.

10 Ndipo Mose ndi Aroni anacita zozizwa izi zonse pamaso pa Farao; koma Yehova analimbitsa mtima wace wa Farao, ndipo sanalola ana a Israyeli aturuke m'dziko lace.

12

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni m'dziko la Aigupto, ndi kuti,

2 Mwezi uno uzikhala kwa inu woyamba wa miyezi; muziuyesa mwezi woyamba wa caka.

3 Mulankhule ndi msonkhano wonse wa Israyeli ndi kuti, Tsiku lakhumi la mwezi uno adzitengere munthu yense mwana wa nkhosa, monga mwa mabanja a atate ao, mwana wa nkhosa pabanja.

4 Banja likaperewera mwana wa nkhosa, munthu ndi mnzace ali pafupi pa nyumba yace atenge monga mwa kufikira kwa anthu ao; muziwerengera mwana wa nkhosa monga mwa kudya kwao.

5 Mwana wa nkhosa wanu azikhala wangwiro, wamwamuna, wa caka cimodzi; muzimtenga ku nkhosa kapena ku mbuzi.

6 Ndipo mukhale naye cisungire kufikira tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi womwe; ndipo bungwe lonse la anthu a Israyeli lizimupha madzulo.

7 Ndipo azitengako mwazi, naupake pa mphuthu za mbali ndi ya pamwamba m'nyumba zimene adyeramo.

8 Ndipo azidya nyamayo usiku womwewo, yooca pamoto, ndi mkate wopanda cotupitsa; aidye ndi ndiwo zowawa,

9 Musaidya yaiwisi, kapena yophika ndi madzi konse ai, koma yooca pamoto; muti wace ndi miyendo yace ndi matumbo ace.

10 Ndipo musasiyako kufikira m'mawa; koma yotsalira kufikira m'mawayo muipsereze ndi moto:

11 Ndipo muziidya cotero: okwinda m'cuuno, nsapato zanu pa mapazi anu ndodo yanu m'dzanja lanu, ndipo muziidya msanga; ndiye Paskha wa Yehova.

12 Pakuti ndidzapita pakati pa dziko la Aigupto usiku womwewo, ndi kukantha ana oyamba onse m'dziko la Aigupto, anthu ndi zoweta; ndipo ndidzacita maweruzo pa milungu yonse ya Aigupto; Ine ndine Yehova.

13 Ndipo mwaziwo udzakhala cizindikilo kwa inu pa nyumba zimene mukhalamo; pamene ndiona mwaziwo ndidzapitirira inu, ndipo sipadzakhala mliri wakukuonongani, pakukantha Ine dziko la Aigupto,

14 Ndipo tsiku lino lidzakhala kwa inu cikumbutso, muzilisunga la madyerero a Yehova; ku mibadwo yanu muzilisunga la madyerero, likhale lemba losatha.

15 Masiku asanu ndi awiri muzidya mkate wopanda cotupitsa; lingakhale tsiku loyamba muzicotsa cotupitsa m'nyumba zanu; pakuti ali yense wakudya mkate wa cotupitsa kuyambira tsiku loyamba kufikira tsiku lacisanu ndi ciwiri, munthu amene adzasadzidwa kwa Israyeli.

16 Ndipo tsiku loyamba kukhale kusonkhana kopatulika, ndi tsiku lacisanu ndi ciwiri kukhalenso kusonkhana kopatulika; pasacitike nchito masikuwo, zokhazi zakudya anthu onse ndizo muzicita.

17 Ndipo muzisunga madyerero a mkate wopanda cotupitsa; pakuti tsiku lomwe lino ndinaturutsa makamu anu m'dziko la Aigupto; cifukwa cace muzisunga tsiku lino m'mibadwo yanu, lemba losatha.

18 Mwezi woyamba, tsiku lace lakhumi ndi cinai madzulo ace, muzidya mkate wopanda cotupitsa, kufikira tsiku la makumi awiri mphambu limodzi la mwezi, madzulo ace.

19 Cisapezeke cotupitsa m'nyumba zanu masiku asanu ndi awiri; pakuti ali yense wakudya kanthu ka cotupitsa, munthuyo adzasadzidwa ku msonkhano wa Israyeli, angakhale ndiye mlendo kapena wobadwa m'dziko.

20 Musadye kanthu ka cotupitsa; mokhala inu monse muzidya mkate wopandacotupitsa.

21 Pamenepo Mose anaitana akuru onse a Israyeli, nanena nao, Pitani, dzitengereni ana a nkhosa monga mwa mabanja anu, nimuphere Paskha.

22 Ndipo muzitenga mpukutu wa hisope, ndi kuubviika m'mwazi uli m'mbale, ndi kupaka mwazi uli m'mbalemo pa mphuthu ya pamwamba ndi pambali; koma inu, asaturuke munthu pakhomo pa nyumba yace kufikira m'mawa.

23 Pakuti Yehova adzapita pakatipo kukantha Aaigupto; koma pamene adzaona mwaziwo pa mphuthu pamwamba ndi za pambali, Yehova adzapitirira pakhomopo, osalola woonongaalowe m'nyumba zanu kukukanthani.

24 Ndipo muzisunga cinthu ici cikhale lemba la kwa inu, ndi kwa ana anu ku nthawi zonse.

25 Ndipo kudzakhala, pamene mulowa m'dziko limene Yehova adzakupatsani, mensa analankhula, muzisunga kutumikira kumeneku.

26 Ndipo kudzakhala, pamene ana anu adzanena ndi inu, Kutumikiraku muli nako nkutani?

27 mudzati, Ndiko nsembe ya Paskha wa Yehova, amene anapitirira nyumba za ana a Israyeli m'Aigupto, pamene anakantha Aaigupto, napulumutsa nyumba zathu.

28 Ndipo anthu anawerama, nalambira. Ndipo ana a Israyeli anamuka nacita monga Yehova adalamulira Mose ndi Aroni; anacita momwemo.

29 Ndipo panakhala pakati pa usiku, Yehova anakantha ana oyamba onse a m'dziko la Aigupto, kuyambira mwana woyamba wa Earao wakukhala pa mpando wacifumu wace kufikira mwana woyamba wa wam'nsinga ali m'kaidi; adi ana oyamba onse a zoweta.

30 Ndipo Farao anauka usiku, iyendi anyamata ace onse, ndi Aaigupto onse; ndipo kunali kulira kwakukulu m'Aigupto; pakuti panalibe nyumba yopanda wakufa m'mwemo.

31 Ndipo anaitana Mose ndi Aroni usiku, nati, Ukani, turukani pakati pa anthu anga, inu ndi ana a Israyeli; ndipo mukani katumikireni Yehova, monga mwanena.

32 Muka nazoni zoweta zanu zazing'ono ndi zazikuru, monga mwanena; cokani, ndi kundidalitsa Inenso.

33 Ndipo Aaigupto anaumiriza anthuwo, nafulumira kuwaturutsa m'dziko; pakuti anati, Tiri akufa tonse.

34 Ndipo anthu anatenga mtanda wao usanatupe, ndi zoumbiramo zao zomangidwa m'zobvala zao pa mapewa ao.

35 Ndipo ana a Israyeli anacita monga mwa mau a Mose; napempha Aaigupto zokometsera zasiliva, ndi zagolidi, ndi zobvala.

36 Ndipo Yehova anapatsa anthu cisomo pamaso pa Aaigupto, ndipo sanawakaniza. Ndipo anawafunkhira Aaigupto.

37 Ndipo ana a Israyeli anayenda ulendo wakucokera ku Ramese kufikira ku Sukoti, zikwi mazana asanu ndi limodzi oyenda okha, ndiwo amuna, osawerenga ana.

38 Ndipo anthu ambiri osokonezeka anakwera nao; ndi nkhosa ndi ng'ombe, zoweta zambirimbiri.

39 Ndipo anaoca timitanda topanda cotupitsa ta mtanda umene anabwera nao ku Aigupto, popeza sadaikamo cotupitsa; pakuti adawapitikitsa ku Aigupto, ndipo sanathe kucedwa, kapena kudzikonzeratu kamba.

40 Ndipo kukhala kwa ana a Israyeli anakhala m'Aigupto ndiko zaka mazana anai kudza makumi atatu.

41 Ndipo kunakhala pakutha zaka mazana anai kudza makumi atatu, inde panakhala tsiku lomwelo, makamu onse a Yehova anaturuka m'dziko la Aigupto.

42 Ndiwo usiku wosungira Yehova ndithu, cifukwa ca kuwaturutsa m'dziko la Aigupto; usiku womwe uno ukhale wosungira Yehova ana onse a Israyeli ku mibadwo yao.

43 Ndipo Yehova anati kwa Mose ndi Aroni, Lemba la Paskha ndi ili: mwana wa mlendo ali yense asadyeko;

44 koma kapolo wa mwini ali yense, wogula ndi ndarama, utamdula, ndipo adyeko.

45 Mlendo kapena wolembedwa nchito asadyeko.

46 Audye m'nyumba imodzi; usaturukira nayo kubwalo nyama yina; ndipo musathyole pfupa lace.

47 Msonkhano wonse wa Israyeli uzicita ici.

48 Koma akakhala nanu mlendo, nakonzera Yehova Paskha, adulidwe amuna ace onse, ndipo pamenepo asendere kuucita; nakhale ngati wobadwa m'dziko; koma wosadulidwa ali yense asadyeko.

49 Pakhale lamulo lomweli pa wobadwa m'dziko, ndi pa mlendo wakukhala pakati pa inu.

50 Ndipo ana onse a Israyeli anacita monga Yehova adawalamulira Mose ndi Aroni, momwemo anacita.

51 Ndipo kunakhala tsiku lomwelo, kuti Yehova anaturutsa ana a Israyeli m'dziko la Aigupto, monga mwa makamu ao.

13

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi kuti,

2 Ndipatulire Ine yense woyamba kubadwa, wotsegulira pa amace mwa ana a Israyeli, mwa anthu ndi mwa zoweta; ndiwo anga.

3 Ndipo Mose ananena ndi anthu, Kumbukirani tsiku linu limene munaturuka m'Aigupto, m'nyumba ya akapolo; pakuti Yehova anakuturutsani muno ndi dzanja lamphamvu; ndipo asadye kanthu ka cotupitsa.

4 Muturuka lero lino mwezi wa Abibu.

5 Ndipo kudzakhala atakulowetsa Yehova m'dziko la Akanani, ndi la Ahiti, ndi la Aamori ndi la Ahivi, ndi la Ayebusi, limene analumbira ndi makolo ako kukupatsa, m'dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi, uzikasunga kutumikira kumeneku mwezi uno.

6 Masiku asanu ndi awiri uzikadya mkate wopanda cotupitsa, ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri likhale la madyerero a Yehova.

7 Azikadya mkate wopanda cotupitsa masiku asanu ndi awiriwo ndipo kasaoneke kanthu ka cotupitsa kwanu; inde cotupitsa cisaoneke kwanu m'malire ako onse.

8 Ndipo ukauze mwana wako wamwamuna tsikulo, ndi kuti, Nditero cifukwa comwe Yehova anandicitira ine poturuka ine m'Aigupto,

9 Ndipo cizikhala ndi iwe ngati cizindikilo pa dzanja lako, ndi cikumbutso pakati pa maso ako; kuti cilamulo ca Yehova cikhale m'kamwa mwako; pakuti Yehova anakuturutsa m'Aigupto ndi dzanja lamphamvu.

10 Cifukwa cace uzikasunga lemba ili pa nyengo yace caka ndi caka.

11 Ndipo kudzakhala, atakulowetsa Yehova m'dziko la Akanani, monga anakulumbirira iwe ndi makolo ako, ndipo anakupatsa ilo,

12 kuti uzikapatulira Yehova onse oyamba kubadwa ndi oyamba onse uli nao odzera kwa zoweta; amunawo ndi a Yehova.

13 Koma woyamba yense wa buru uzimuombola ndi mwana wa nkhosa; ndipo ukapanda kumuombola uzimthyola khosi; koma oyamba onse a munthu mwa ana ako uziwaombola.

14 Ndipo kudzakhala, akakufunsa mwana wako masiku akudzawo ndi kuti, Ici nciani? ukanene naye, Yehova anatiturutsa m'Aigupto, m'nyumba ya aka polo, ndi dzanja lamphamvu;

15 ndipo kunakhala, pamene Farao anadziumitsa kuti tisamuke, Yehova anawapha onse oyamba kubadwa m'dziko la Aigupto, kuyambira oyamba a anthu, kufikira oyamba a zoweta; cifukwa cace ndimphera nsembe Yehova zazimuna zoyamba kubadwa zonse; koma oyamba onse a ana anga ndiwaombola.

16 Ndipo cizikhala ngati cizindikilo pa dzanja lako, ndi capamphumi pakati pa maso ako; pakuti Yehova anatiturutsa m'Aigupto ndi dzanja lamphamvu.

17 Ndipo kunakhala pamene Farao adalola anthu amuke, Mulungu sanawatsogolera njira ya dziko la Afilisti, ndiyo yaifupi; pakuti Mulungu anati. Angadodome anthuwo pakuona nkhondo ndi kubwerera m'mbuyo kumka ku Aigupto.

18 Koma Mulungu anawazungulitsa anthuwo, ku njira ya kucipululu ya Nyanja Yofiira; ndipo ana a Israyeli anakwera kucokera m'dziko la Aigupto okonzeka.

19 Ndipo Mose anamuka nao mafupa a Yosefe; pakuti adawalumbiritsatu ana a Israyeli ndi kuti, Mulungu adzakuzondani ndithu ndipo mukakwere nao mafupa anga osawwya kuno.

20 Ndipo anacokera ku Sukoti, nagona ku Etamu, pa malekezero a cipululu.

21 Ndipo Yehova anawatsogolera usana ndi mtambo njo kuwatsogolera m'njira; ndi usiku ndi moto njo, wakuwawalitsira; kuti ayende usana ndi usiku;

22 sanacotsa mtambo usana, kapena mtambo wamoto usiku, pamaso pa anthu.

14

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2 Lankhula ndi anthu a Israyeli kuti abwerere m'mbuyo nagone patsogolo pa Pihahiroti, pakati pa Migidoli ndi nyanja yamcere, patsogolo pa Baala-Zefoni; pandunji pace mugone panyanja.

3 Ndipo Farao adzanena za ana a Israyeli, Azimidwa dziko, cipululu cawatsekera.

4 Ndipo ndidzalimbitsa mtima wace wa Farao kuti awalondole; ndipo ndidzalemekezedwa pa Farao ndi pa nkhondo yace yonse; pamenepo Aaigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, Ndipo anacita comweco.

5 Ndipo anauza mfumu ya Aigupto kuti anthu adathawa; ndi mtima wa Farao ndi wa anyamata ace inasandulikira anthuwo, ndipo anati, Ici nciani tacita, kuti talola Israyeli amuke osatigwiriranso nchito?

6 Ndipo anamanga gareta lace, napita nao anthu ace;

7 napita nao magareta osankhika mazana asanu ndi limodzi, ndi magareta onse a m'Aigupto, ndi akapitao ao onse.

8 Ndipo Yehova analimbitsa mtima wa Farao, mfumu ya Aigupto, ndipo iye analondola ana a Israyeli; koma ana a Israyeli adaturuka ndi dzanja lokwezeka.

9 Ndipo Aaigupto anawalondola, ndiwo akavalo ndi magareta onse a Farao, ndi apakavalo ace, ndi nkhondo yace, nawapeza ali kucigono kunyanja, pa Pihahiroti, patsogolo pa Baala-Zefoni.

10 Ndipo pamene Farao anayandikira ana a Israyeli anatukula maso ao, taonani, Aaigupto alinkutsata pambuyo pao; ndipo anaopa kwambiri; ndi ana a Israyeli anapfuulira kwa Yehova.

11 Ndipo anati kwa Mose, Kodi mwaticotsera kuti tikafe m'cipululu cifukwa panahbe manda m'Aigupto? Nciani ici mwaticitira kuti mwatiturutsa m'Aigupto?

12 Si awa maowo tinalankhula nanu m'Aigupto ndi kuti, Tliekeni, kuti tigwirire nchito Aaigupto? pakuti kutumikira Aaigupto kutikomera si kufa m'cipululu ai.

13 Ndipo Mose ananena ndi anthu, Musaope, cirimikani, ndipo penyani cipulumutso ca Yehova, cimene adzakucitirani lero; pakuti Aaigupto mwawaona lerowa simudzawaonansokonse.

14 Yehova adzakugwirirani nkhondo, ndipo inu mudzakhala cere.

15 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Upfuuliranji kwa Ine? lankhula ndi ana a Israyeli kuti aziyenda.

16 Ndipo iwe nyamula ndodo yako, nutambasulire dzanja lako kunyanja, nuigawe, kuti ana a Israyeli alowe pakati pa nyanja pouma.

17 Ndipo Ine, taonani, ndilimbitsa mitima ya Aaigupto, kuti alowemo powatsata; ndipo ndidzalemekezedwa pa Farao, ndi pa nkhondo yace yonse, pa magareta ace, ndi pa okwera pa akavalo ace.

18 Ndipo Aaigupto adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, polemekezedwa Ine pa Farao, pa magareta ace, ndi pa okwera pa akavalo ace.

19 Ndipo mthenga wa Mulungu, wakutsogolera ulendo wa Israyeli, unacokako, nutsata pambuyo pao; ndipo mtambo njo uja unacoka patsogolo pao, nuima pambuyo pao;

20 nulowa pakati pa ulendo wa Aaigupto ndi ulendo wa Aisrayeli ndipo mtambo unacita mdima, komanso unaunikira usiku; ndipo ulendo wina sunayandikizana ndi unzace usiku wonse.

21 Ndipo Mose anatambasulira dzanja lace kunyanja; ndipo Yehova anabweza nyanja ndi mphepo yolimba ya kum'mawa usiku wonse, naumitsa nyanja; ndipo madziwo anagawikana.

22 Ndipo ana a Israyeli analowa pakati pa nyanja pouma; ndi madziwo anakhala kwa iwo ngati khoma palamanja, ndi palamanzere.

23 Ndipo Aaigupto anawalondola, nalowa pakati pa nyanja powatsata, ndiwo akavalo onse a Farao, magareta ace, ndi apakavalo ace.

24 Ndipo kunali, ulonda wa mamawa, Yehova ali m'moto ndi m'mtambo njo anapenyera pa ulendo wa Aaigupto, Baubvuta ulendo wa Aaigupto.

25 Ndipo anagurula njinga za magareta ao, nawayendetsa molemetsa; pamenepo Aaigupto anati, Tithawe pamaso pa Israyeli; pakuti Yehova alikuwagwirira nkhondo pa Aaigupto.

26 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tambasulira dzanja lako kunyanja, kuti madziwo abwerere kudzamiza Aaigupto, magareta ao, ndi apakavalo ao.

27 Ndipo Mose anatambasulira dzanja lace kunyanja, ndi nyanja inabwerera m'mayendedwe ace mbanda kuca; ndipo Aaigupto pothawa anakomana nayo; ndipo Yehova anakutumula Aaigupto m'kati mwa nyanja.

28 Popeza madziwo anabwerera, namiza magareta ndi apakavalo, ndiwo nkhondo yonse ya Farao imene idalowa pambuyo pao m'nyanja; sanatsala wa iwowa ndi mmodzi yense.

29 Koma ana a Israyeli anayenda pouma pakati pa nyanja; ndi madziwo anakhala ngati khoma kwa iwo, palamanja ndi palamanzere.

30 Comweco Yehova anapulumutsa Israyeli tsiku lomwelo m'manja a Aaigupto; ndipo Israyeli anaona Aaigupto akufa m'mphepete mwa nyanja.

31 Ndipo Israyeli anaiona nchito yaikuru imene Yehova anacitira Aaigupto, ndipo anthuwo anaopa Yehova; nakhulupirira Yehova ndi mtumiki wace Mose.

15

1 Nyimbo yolemekeza Mulungu, Pamenepo Mose ndi ana a Israyeli anayimbira Yehova nyimbo iyi, nanena, ndi kuti, Ndidzayimbira Yehova pakuti wapambanatu; Kavalo ndi wokwera wace anawaponya m'nyanja.

2 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Ndipo wakhala cipulumutso canga; Ameneyo ndiye Mulungu wanga, ndidzamlemekeza: Ndiye Mulungu wa kholo langa, ndidzammveketsa.

3 Yehova ndiye wankhondo; Dzina lace ndiye Yehova.

4 Magareta a Farao ndi nkhondo yace anawaponya m'nyanja; Ndi akazembe ace osankhika anamira m'Nyanja Yofiira.

5 Nyanja inawamiza: Anamira mozama ngati mwala.

6 Dzanja lanu lamanja, Yehova, lalemekezedwa ndi mphamvu, Dzanja lanu lamanja, Yehova, laphwanya mdani.

7 Ndipo ndi ukulu wanu waukuru mwapasula akuukira Inu; Mwatumiza mkwiyo wanu, unawanyeketsa ngati ciputu.

8 Ndipondi mpumo wa m'mphuno mwanu madzi anaunjikika, Mayendedwe ace anakhala ciriri ngati mulu; Zozama zinalimba m'kati mwa nyanja.

9 Mdani anati, Ndiwalondola, ndiwakumika, ndidzagawa zofunkha; Ndidzakhuta nao mtima; Ndidzasolola lupanga langa, dzanja langa lidzawaononga.

10 Munaombetsa mphepo yanu, nyanja inawamiza; Anamira m'madzi akuru ngati mtobvu.

11 Manana ndi Inu ndani mwa milungu, Yehova? Manana ndi Inu ndani, wolemekezedwa, woyera, Woopsa pomyamika, wakucita zozizwa?

12 Mwatambasula dzanja lanu lamanja, Nthaka inawameza,

13 Mwa cifundo canu mwatsogolera anthu amene mudawaombola; Mwa mphamvu yanu mudawalondolera njira yakumka pokhala panu poyera.

14 Mitundu ya anthu idamva, inanthunthumira; Kuda mtima kwagwira anthu okhala m'Filistiya.

15 Pamenepo mafumu a Edomu anadabwa; Agwidwa nako kunthunthumira amphamvu a ku Moabu; Okhala m'Kanani onse asungunukamtima.

16 Kuopa kwakukuru ndi mantha ziwagwera; Pa dzanja lanu lalikuru akhala cete ngati mwala; Kufikira apita anthu anu, Yehova, Kufikira apita anthu amene mudawaombola.

17 Mudzawafikitsa, ndi kuwaoka pa phiri la colowa canu, Pamalo pamene munadzipangira mukhalepo, Yehova, Malo oyera, amene manja anu, Ambuye, adakhazikika.

18 Yehova adzacita ufumu nthawi yomka muyaya.

19 Pakuti akavalo a Farao analowa m'nyanja, ndi magareta ace ndi apakavalo ace, ndipo Yehova anawabwezera madzi a m'nyanja; koma ana a Israyeli anayenda pouma pakati pa nyanja.

20 Ndipo Miriamu mneneriyo, mlongo wa Aroni, anagwira lingaka m'dzanja lace; ndipo akazi onse anaturuka kumtsata ndi malingaka ndi kuthira mang'ombe.

21 Ndipo Miriamu anawayankha, Yimbirani Yehova, pakuti wapambanatu; Kavalo ndi wokwera wace anawaponya m'nyanja. Madzi a ku Mara.

22 Ndipo Mose anatsogolera Israyeli kucokera ku Nyanja Yofiira, ndipo anaturukako nalowa m'cipululu ca Suri; nayenda m'cipululu masiku atatu, osapeza madzi.

23 Pamene anafika ku Mara, sanakhoza kumwa madzi a Mara, pakuti anali owawa; cifukwa cace anacha dzina lace Mara.

24 Ndipo anthu anadandaulira Mose, ndi kuti, Tidzamwa ciani?

25 Ndipo iye anapfuulira kwa Yehova; ndipo Yehova anamsonyeza mtengo ndipo anauponya m'madzimo, ndi madzi anasanduka okoma. Pamenepo anawapangira lemba ndi ciweruzo, ndi pomwepa anawayesa;

26 ndipo anati, Ngati udzamveratu mau a Yehova, Mulungu wako, ndi kucita zoona pamaso pace, ndi kuchera khutu pa malamulo ace, ndi kusunga malemba ace onse, za nthenda zonse ndinaziika pa Aaigupto sindidzaziika pa iwe nnena imodzi; pakuti Ine Yehova ndine wakuciritsa iwe.

27 Ndipo anafika pa Elimu, ndi pamenepo panali akasupe a madzi khumi ndi awiri, ndi akanjedza makumi asanu ndi awiri; ndipo anamanga cigono cao pomwepo pa madziwo.

16

1 Ndipo anacoka ku Elimu, ndi khamu lonse la ana a Israyeli linalowa m'cipululu ca Sini, ndico pakati pa Elimu ndi Sinai, tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi waciwiri ataturuka m'dziko la Aigupto.

2 Ndipo khamu lonse la ana a Israyeli linadandaulira Mose ndi Aroni m'cipululu;

3 nanena nao ana a Israyeli, Ha! mwenzi titafa ndi dzanja la Yehova m'dziko la Aigupto, pokhala ife pa miphika ya nyama, pakudya mkate ife cokhuta; pakuti mwatiturutsa kudza nafe m'cipululu muno kudzapha msonkhano uwu wonse ndi njala.

4 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Taona, ndidzabvumbitsira inu mkate wodzera kumwamba; ndipo anthu azituruka ndi kuola muyeso wa tsiku pa tsiku lace, kuti ndiwayese, ngati ayenda m'cilamulo canga kapena iai.

5 Ndipo kudzakhala tsiku lacisanu ndi cimodzi, kuti azikonza umene adabwera nao, ataoniezapo muyeso unzace wa pa tsiku limodzi.

6 Ndipo Mose ndi Aroni ananena ndi ana onse a Israyeli, Madzulo mudzadziwa kuti Yehova anakuturutsani m'dziko la Aigupto;

7 ndi m'mawa mwace mudzaona ulemerero wa Yehova, popeza alinkumva mulikudandaulira Yehova; pakuti ife ndife ciani, kuti mutidandaulira ife?

8 Nanenanso Mose, Pakukupatsani Yehova nyama ya kudya madzulo, ndi mkate wokhuta m'mawa, atero popeza Yehova adamva madandaulo anu amene mumdandaulira nao. Koma ife ndife ciani? simulikudandaulira ife koma Yehova.

9 Ndipo Mose anati kwa Aroni, Nena ndi khamu lonse la ana a Israyeli, Yandikizani pamaso pa Yehova, pakuti anamva madandaulo anu.

10 Ndipo kunakhala, pakunena Aroni ndi khamu lonse la ana a Israyeli kuti iwo anatembenukira kucipululu, ndipo, taonani, ulemerero wa Yehova unaoneka mumtambo.

11 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

12 Ndamva madandaulo a ana a Israyeli; lankhula nao ndi kuti, Madzulo mudzadya nyama, ndi m'mawa mudzakhuta mkate; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

13 Ndipo kunali madzulo zinakwera zinziri, ndipo zinakuta tsasa, ndi m'mawa padagwa mame pozungulira tsasa.

14 Ndipo atasansuka mame adagwawo, taonani, pankhope pa cipululu pali kanthu kakang'ono kamphumphu, kakang'ono ngati cipale panthaka.

15 Ndipo pamene ana a Israyeli anakaona, anati wina ndi mnzace, Nciani ici? pakuti sanadziwa ngati nciani. Ndipo Mose ananena nao, Ndiwo mkatewo Yehova wakupatsani ukhale cakudya canu,

16 Amenewo ndiwo mau walamulira Yehova, Aoleko yense monga mwa njala yace; munthu mmodzi omeri limodzi, monga momwe muli, yense atengere iwo m'hema mwace.

17 Ndipo ana a Israyeli anatero, naola wina wambiri, wina pang'ono.

18 Ndipo pamene anayesa ndi omeri, iye amene adaola wambiri sunamtsalira, ndi iye amene adaola pang'ono sunamsowa; yense anaola monga mwa njala yace.

19 Ndipo Mose ananena nao, Palibe munthu asiyeko kufikira m'mawa.

20 Koma sanammvera Mose; ndipo ena anasiyako kufikira m'mawa; koma unagwa mphutsi, nununkha. Ndipo Mose anakwiya nao.

21 Ndipo anauola m'mawa ndi m'mawa, yense monga mwa njala yace; popeza likatentha dzuwa umasungunuka.

22 Ndipo kunali tsiku lacisanu ndi cimodzi, anaola mkate, naonjezapo linzace, maomeri awiri pa munthu mmodzi; ndipo akazembe a khamulo anadza nauza Mose.

23 Ndipo ananena nao, Ici ndi comwe Yehova analankhula, Mawa ndiko kupuma, Sabata lopatulika la Yehova; cimene muzioca, ocani, ndi cimene muziphika phikani; ndi cotsala cikukhalireni cosunguka kufikira m'mawa.

24 Ndipo anausunga kufikira m'mawa, monga adalamulira Mose; koma sunanunkha, ndipo sunagwa mphutsi.

25 Ndipo Mose anati, Muudye lero; pakuti lero ndilo Sabata la Yehova; simuupeza lero pabwalo.

26 Muziola uwu masiku asanu ndi limodzi; koma tsiku lacisanu ndi ciwiri ndilo la Sabata, pamenepo padzakhala palibe.

27 Ndipo kunali tsiku la Sabata, kuti anthu ena anaturuka kukaola, koma sanaupeza.

28 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Mukana kusunga zouza zanga ndi malamulo anga kufikira titi?

29 Taonani, popeza Yehova anakupatsani Sabata, cifukwa cace tsiku lacisanu ndi cimodzi alikupatsa inu mkate wofikira masiku awiri; khalani yense m'malo mwace, munthu asaturuke m'malo mwace tsiku lacisanu ndi ciwiri.

30 Ndipo anthu anapumula tsiku lacisanu ndi ciwiri.

31 Ndipo mbumba ya Israyeli inaucha dzina lace Mana; ndiwo ngati zipatso zampasa, oyera; powalawa akunga timitanda tosanganiza ndi uci.

32 Ndipo Mose anati, Awa ndi mau anauza Yehova, Dzazani omeri nao, asungikire mibadwo yanu; kuti aone mkatewo ndinakudyetsani nao m'cipululu, muja ndinakuturutsani m'dziko la Aigupto.

33 Ndipo Mose anati kwa Aroni, Tenga mphika, nuthiremo mana odzala omeri, nuuike pamaso pa Yehova, usungikire mibadwo yanu.

34 Monga Yehova anauza Mose, momwemo Aroni anauika patsogolo pa Mboni, usungikeko.

35 Ndipo ana a Israyeli anadya mana zaka makumi anai, kufikira atalowa dziko la midzi; anadya mana kufikira analowa malire a dziko la Kanani.

36 Koma omeri ndilo limodzi la magawo khumi la efa.

17

1 Ndipo khamu lonse la ana a Israyeli linacoka m'cipululu ca Sini, m'zigono zao, monga mwa mau a Yehova, nagona m'Refidimu. Koma kumeneko kunalibe madzi akumwa anthu.

2 Pamenepo anthu anatsutsana ndi Mose, nati, Tipatseni madzi timwe, Koma Mose ananena nao, Mutsutsana nane bwanji? Muyeseranji Yehova?

3 Ndipo pomwepo anthu anamva ludzu lokhumba madzi; ndi anthu anadandaulira Mose, nati, Munatikwezeranji kucokera ku Aigupto, kudzatipha ife ndi ana athu ndi zoweta zathu ndi ludzu?

4 Ndipo Mose anapfuulira kwa Yehova, ndi kuti, Ndiwacitenji anthuwa? andilekera pang'ono kundiponya miyala.

5 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Pita pamaso pa anthu, nutenge pamodzi nawe akuru ena a Israyeli; nutenge m'dzanja mwako ndodo ija unapanda nayo nyanja, numuke.

6 Taona, ndidzaima pamaso pako pathanthwe m'Horebe; ndipo upande thanthwe, nadzaturukamo madzi, kuti anthu amwe. Ndipo Mose anacita comweco pamaso pa akuru a Israyeli.

7 Ndipo anacha dzina la malowo Masa, ndi Meriba, cifukwa ca kutsutsana kwa ana a Israyeli; popezanso anayesa Yehova, ndi kuti, Kodi Yehova ali pakati pa ife, kapena iai?

8 Pamenepo anadza Amaleki, nayambana ndi Israyeli m'Refidimu.

9 Ndipo Mose anati kwa Yoswa, Utisankhulire amuna, nuturuke kuyambana naye Amaleki; mawa ndidzaima pamwamba pa citunda, ndi ndodo ya Mulungu m'dzanja langa.

10 Ndipo Yoswa anacita monga Mose adanena naye, nayambana ndi Amaleki; ndipo Mose, ndi Aroni, ndi Huri anakwera pamwamba pa citunda.

11 Ndipo kunakhala, pamene Mose anakweza dzanja lace Israyeli analakika; koma pamene anatsitsa dzanja lace Amaleki analakika.

12 Koma manja a Mose analema; ndipo anatenga mwala, nauika pansi pa iye, nakhala pamenepo; ndipo Aroni ndi Huri anagwiriziza manja ace, wina mbali yina, wina mbali yina; ndi manja ace analimbika kufikira litalowa dzuwa.

13 Ndipo Yoswa anatyola Amaleki ndi anthu ace ndi kuukali kwa lupanga.

14 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Lembera ici m'buku, cikhale cikumbutso, nucimvetse Yoswa; kuti ndidzafafaniza konse cikumbukilo ca Amaleki pansi pa thambo.

15 Ndipo Mose anamanga guwa la nsembe, nalicha dzina lace Yehova Nisi:

16 nati, Yehova walumbira: padzakhala nkhondo ya Yehova pa Amaleki m'mibadwo mibadwo.

18

1 Ndipo Yetero, wansembe wa Midyani, mpongozi wa Mose, anamva zonse zimene Mulungu adacitira Mose ndi Israyeli anthu ace, kuti Yehova adaturutsa Israyeli m'Aigupto.

2 Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose, anabwera naye Zipora mkazi wa Mose (atamtuma kwao), ndi ana ace awiri;

3 dzina la winayo ndiye Gerisomu, pakuti anati, Ndakhala mlendo m'dziko lacilendo;

4 ndi dzina la mnzace ndiye Eliezere; pakuti anati, Mulungu wa kholo langa anakhala thandizo langa nandilanditsa ku lupanga la Farao.

5 Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose, anadza ndi ana ace amuna ndi mkazi wace kwa Mose kucipululu kumene adamangako, pa phiri la Mulungu;

6 nati kwa Mose, Ine mpongozi wako Yetero ndadza kwa iwe, ndi mkazi wako, ndi ana ace omwe awiri.

7 Ndipo Mose anaturuka kukakomana ndi mpongozi wace, nawerama, nampsompsona; nafunsana ali bwanji, nalowa m'hema.

8 Ndipo Mose anafotokozera mpongozi wace zonse Yehova adazicitira Farao ndi Aaigupto cifukwa ca Israyeli; ndi mabvuto onse anakomana nao panjira, ndi kuti Yehova adawalanditsa.

9 Ndipo Yetero anakondwera cifukwa ca zabwino zonse Yehova adazicitira Israyeli, ndi kuwalanditsa m'dzanja la Aaigupto.

10 Nati Yetero, Woyamikika Yehova, amene anakulanditsani m'dzanja la Aaigupto, ndi m'dzanja la Farao; ameneanalanditsa anthu awa pansi pa dzanja la Aaigupto.

11 Tsopano ndidziwa kuti Yehova ali wamkuru ndi milungu yonse; pakuti momwe anadzikuza okha momwemo anawaposa,

12 Ndipo Yetero, mpongozi wa Mose, anamtengera Mulungu nsembe Yopsereza, ndi nsembe zophera; ndipo Aroni ndi akuru onse a Israyeli anadza kudzadya mkate ndi mpongozi wa Mose pamaso pa Mulungu.

13 Ndipo kunatero kuti m'mawa mwace Mose anakhala pansi kuweruzira anthu mirandu yao; ndipo anthu anakhala ciriri pamaso pa Mose kuyambira m'mawa kufikira madzulo.

14 Ndipo pamene mpongozi wace wa Mose anaona zonsezi iye anawacitira anthu, anati, Cinthu ici nciani uwacitira anthuci? Umakhala pa wekha bwanji, ndi anthu onse amakhala ciriri pamaso pako kuyambira m'mawa kufikira madzulo?

15 Ndipo Moce anati kwa mpongozi wace, Cifukwa anthu amadza kwa ine kudzafunsira Mulungu;

16 akakhala nao mlandu adza kwa ine, kuti ndiweruze pakati pa munthu ndi mnansi wace, ndi kuti ndiwadziwitsemalemba a Mulungu, ndi malamulo ace.

17 Koma mpongozi wa Mose ananena naye, Cinthu ucitaci siciri cabwino ai.

18 Udzalema konse, iwe ndi anthu amene uli nao; pakuti cikulaka cinthu ici; sungathe kucicita pa wekha.

19 Tamvera mau anga tsopano, ndikupangire nzeru, ndi Mulungu akhale nawe; ukhale m'malo mwa anthu kwa Mulungu, nupite nayo mirandu kwa Mulungu;

20 nuwamasulire malemba, ndi malamulo, ndi kuwadziwitsa njira imene ayenera kuyendamo, ndi nchito imene ayenera kucita.

21 Koma iwe, dzisankhire mwa anthu ako onse, amuna amtima, akuopa Mulungu, amuna oona, akudana nalo phindu la cinyengo; nuwaikire iwo oterewa, akuru a pa zikwi, akuru a pa mazana, akuru a pa makumi asanu, akuru a pa makumi;

22 ndipo iwo aweruze mirandu ya anthu nthawi zonse; ndipo kudzakhala kuti mirandu yaikuru yonse abwere nayo kwa iwe; koma mirandu yaing'ono yonse aweruze okha; potero idzakucepera nchito, ndi iwo adzasenza nawe.

23 Ukacite cinthuci, ndi Mulungu akakuuza cotero, udzakhoza kupirira, ndi anthu awa onse adzapita kwao mumtendere.

24 Ndipo Mose anamvera mau a mpongozi wace, nacita zonse adazinena.

25 Ndipo Mose anasankha amuna amtima mwa Aisrayeli onse, nawaika akuru a pa anthu, akuru a pa zikwi, akuru a pa mazana, akuru a pa makumi asanu, ndi akuru a pa makumi.

26 Ndipo anaweruza anthu nthawi zonse; mlandu wakuwalaka amabwera nao kwa Mose, ndi milandu yaing'ono yonse amaweruza okha.

27 Ndipo Mose analola mpongozi wace amuke; ndipo anacoka kumka ku dziko lace.

19

1 Mwezi wacitatu ataturuka ana a Israyeli m'dziko la Aigupto, tsiku lomwelo, analowa m'cipululu ca Sinai.

2 Pakuti anacoka ku Refidimu, nalowa m'cipululu ca Sinai, namanga tsasa m'cipululumo; ndipo Israyeli anamanga tsasa pamenepo pandunji pa phirilo.

3 Ndipo Mose anakwera kwa Mulungu; ndipo Yehova ali m'phirimo anamuitana, ndi kuti, Uzitero kwa mbumba ya Yakobo, nunene kwa ana a Israyeli, kuti,

4 Inu munaona cimene ndinacitira Aaigupto; ndi kuti ndanyamula inu monga pa mapiko a mphungu, ndi kubwera nanu kwa Ine ndekha.

5 Ndipo tsopano, ngati mudzamvera mau anga ndithu, ndi kusunga cipangano canga, ndidzakuyesani cuma canga ca padera koposa mitundu yonse ya anthu; pakuti dziko lonse lapansi ndi langa;

6 ndipo ndidzakuyesani ufumu wanga wa ansembe, ndi mtundu wopatulika. Awa ndi mau amene ukalankhule ndi ana a lsrayeli.

7 Ndipo Mose anadza, naitana akuru a anthu, nawaikira pamaso pao mau awa onse amene Yehova adamuuza.

8 Ndipo anthu onse anabvomera pamodzi, nati, Zonse adazilankhula Yehova tidzazicita. Ndipo Mose anabwera nao mau a anthu kwa Yehova.

9 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Taona, ndikudza kwa iwe mu mtambo wakuda bii, kuti anthu amve pamene ndilankhula ndi iwe, ndi kuti akubvomereze nthawi zonse. Pakuti Mose adauza Yehova mau a anthuwo.

10 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Muka kwa anthuwo, nuwapatulitse lero ndi mawa, ndipo atsuke zobvala zao,

11 nakonzekeretu tsiku lacitatu; pakuti tsiku lacitatu Yehova adzatsika pa phiri la Sinai pamaso pa anthu onse.

12 Ndipo ukalembere anthu malire pozungulira, ndi kuti, Muzicenjera musakwere m'phiri, musakhudza cilekezero cace; wokhudza phirilo adzaphedwa ndithu;

13 dzanja liri lonse lisalikhudze, wakulikhudza azimponyatu miyala, kapena kumpyoza; ngakhale coweta ngakhale munthu, zisakhale ndi moyo. Pamene lipenga libanika liu lace azikwera m'phirimo.

14 Ndipo Mose anatsika m'phiri kumka kwa anthu, nawapatulitsa anthu; natsuka iwo zobvala zao.

15 Ndipo anati kwa anthu, Mukonzekeretu tsiku lacitatu nimusayandikiza mkazi.

16 Ndipo kunali tsiku lacitatu, m'mawa, panali mabingu ndi zimphezi, ndi mtambo wakuda bii paphiripo, ndi liu la lipenga lolimbatu; ndi anthu onse okhala kutsasa ananjenjemera.

17 Ndipo Mose anaturutsa anthu kutsasa, kuti akomane ndi Mulungu; ndipo anaima patsinde pa phiri.

18 Ndipo phiri la Sinai linafuka monsemo, popeza Yehova anatsikira m'moto pamenepo; ndi utsi wace unakwera ngati utsi wa m'ng'anjo, ndi phiri lonse linagwedezeka kwambiri,

19 Ndipo pamene liu la lipenga linamveka linakulira-kulira, Mose ananena, ndi Mulungu anamyankha ndi mau.

20 Ndipo Yehova anatsikira pa phiri la Sinai, pamutu pace pa phiri; ndipo Yehova anaitana Mose akwere pamutu pa phiri; ndi Mose anakwerapo.

21 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tsika, cenjeza anthu, kuti angapyolere kwa Yehova kudzaona, ndipo angagwe ambiri a iwowa.

22 Ansembenso, akuyandikiza kwa Yehova adzipatulitse, angawapasule Yehova.

23 Ndipo Mose anati kwa Yehova, Anthu sangathe kukwera m'phiri la Sinai; pakuti Inu mwaticenjeza, ndi kuti, Lemba malire m'phirimo, ndi kulipatula.

24 Ndipo Yehova anati kwa iye, Muka, tsika: nukwere iwe ndi Aroni pamodzi ndi iwe; koma ansembe ndi anthu asapyole kukwera kwa Yehova, angawapasule.

25 Pamenepo Mose anawatsikira anthu, nanena nao.

20

1 Ndipo Mulungu ananena mau onse amenewa, nati:

2 INE ndine YEHOVA Mulungu wako, amene ndinaturutsa iwe ku dziko la Aigupto, ku nyumba ya akapolo.

3 Usakhale nayo milungu yina koma Ine ndekha.

4 Usadzipangire iwe wekha fano losema, kapena cifaniziro ciri conse ca zinthu za m'thambo la kumwamba, kapena za m'dziko lapansi, kapena za m'madzi a pansi pa dziko;

5 usazipembedzere izo, usazitumikire izo; cifukwa Ine Yehova Mulungu wako ndiri Mulungu wansanje, wakulanga ana cifukwa ca atate ao, kufikira mbadwo wacitatu ndi wacinai wa iwo amene akudana ndi Ine;

6 ndi kuwacitira cifundo anthu zikwizikwi a iwo amene akondana ndi Ine, nasunga malamulo anga.

7 Usaehule dzina la Yehova Mulungu wako pacabe; cifukwa Yehova sadzamuyesa iye wosacimwa, amene achula pacabe dzina lacelo.

8 Uzikumbukila tsiku la Sabata, likhale lopatulika.

9 Masiku asanu ndi limodzi uzigwira, ndi kumariza nchito zako zonse;

10 koma tsiku lacisanu ndi ciwiri ndilo Sabata la Yehova Mulungu wako; usagwire nchito iri yonse, kapena iwe wekha, kapena mwana wako wamwamuna, kapena mwana wako wamkazi, kapena wanchito wako wamwamuna, kapena wanchito wako wamkazi, kapena nyama zako, kapena mlendo amene ali m'mudzi mwako;

11 cifukwa masiku asanu ndi limodzi Yehova adamariza zakumwamba ndi zapansi, ndi nyanja, ndi zinthu zonse ziri m'menemo, napumula tsiku ladsanu ndi ciwiri; cifukwa cace Yehova anadalitsa tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika.

12 Uzilemekeza atate wako ndi amako; kuti acuruke masiku ako m'dziko limene Yehova Mulungu wako akupatsa iwe.

13 Usaphe.

14 Usacite cigololo.

15 Usabe.

16 Usamnamizire mnzako.

17 Usasirire nyumba yace ya mnzako, usasirire mkazi wace wa mnzako, kapena wanchito wace wamwamuna, kapena wanchito wace wamkazi, kapena ng'ombe yace, kapena buru wace, kapena kanthu kali konse ka mnzako.

18 Ndipo anthu onse anaona mabingu ndi zimphezi, ndi liu la lipenga, ndi phiri lirikufuka; ndipo pamene anthu anaziona, ananjenjemera, naima patali.

19 Ndipo anati kwa Mose, Mulankhule nafe ndinu, ndipo tidzamva; koma asalankhule nafe Mulungu, kuti tingafe,

20 Ndipo Mose anati kwa anthu, Musaope; pakuti Mulungu wadza kukuyesani ndi kuti kumuopa iye kukhale pamaso panu, kuti musacimwe.

21 Ndipo anthu anaima patali, koma Mose anayandikiza ku mdima waukuru kuli Mulungu.

22 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Uzitero ndi ana a Israyeli, kuti, Mwapenya nokha kuti ndalankhula nanu, kucokerakumwamba.

23 Musapange milungu yasiliva ikhale pamodzi ndi Ine; musadzipangire milungu yagolidi.

24 Undiumbire guwa la nsembe ladothi, nundiphere pomweponsembe zako zopsereza, ndi nsembe zako zamtendere, nkhosa zako ndi ng'ombe zako; pali ponse ndikumbukiritsa anthu dzina langa ndidzakudzera ndi kukudalitsa.

25 Ndipo ukandimangira guwa la nsembe lamiyala, usalimanga ndi miyala yosema; ukakwezapo cosemera cako, waliipsa.

26 Kapena usakwere ndi makwerero ku guwa langa la nsembe, kuti angaoneke marisece ako pamenepo.

21

1 Ndipo awa ndiwo maweruzo amene uziika pamaso pao.

2 Ukagula mnyamata Mhebri, azigwira nchito zaka zisanu ndi cimodzi; koma cacisanu ndi ciwiri azituruka waufulu cabe.

3 Akalowa ali yekha azituruka ali yekha; akakhala ndi mkazi, mkazi wace azituruka naye.

4 Akampatsa mkazi mbuye wace, ndipo akambalira ana amuna ndi akazi, mkaziyo ndi ana ace azikhala a mbuye wace, ndipo azituruka ali yekha.

5 Koma mnyamatayo akanenetsa, Ndikonda mbuye wanga, mkazi wanga, ndi ana anga; sindituruka waufulu;

6 pamenepo mbuye wace azifika naye kwa oweruza, nafike naye kukhomo, kapena kumphuthu, ndipo mbuye wace amboole khutu lace ndi lisungulu; ndipo iye azimgwirira nchito masiku onse.

7 Ndipo munthu akagulitsa mwana wace wamkazi akhale mdzakazi, iyeyo asaturuke monga amaturuka anyamata.

8 Akapanda kumkonda mbuye wace, amene anamtoma mwini yekha, azilola kuti amuombole; alibe mphamvu yakumgulitsa kwa anthu acilendo, popeza wacita naye monyenga.

9 Koma ngati amtomera mwana wace wamwamuna, amcitire monga kuyenera ana akazi.

10 Akamtengera mkazi wina, asacepetse cakudya cace, zobvala zace, ndi za ukwati zace zace.

11 Ndipo akapanda kumcitira izi zitatu, azituruka cabe, osaperekapo ndalama.

12 Iye amene akantha munthu kotero kuti wafa, aphedwe ndithu.

13 Koma akapanda kumlalira, koma Mulungu akalola akomane ndi mnzace, ndidzakuikirani pothawirapo iye.

14 Koma munthu akacita dala pa mnzace, kumupha monyenga; uzimcotsa ku guwa langa la nsembe, kuti afe.

15 Munthuwakukanthaatatewace, kapena amai wace, aphedwe ndithu.

16 Iye wakuba munthu, angakhale wamgulitsa, kapena akampeza m'dzanja lace, aphedwe ndithu.

17 Munthu wakutemberera atate wace, kapena amai wace, aphedwe ndithu.

18 Akalimbana amuna, ndipo wina akakantha mnzace ndi mwala, kapena ndi nkhonyo, wosafa iye, koma wakhulungira pakama;

19 akaukanso, nakayendayenda pabwalo ndi ndodo yace, womkanthayo azikhala womasuka; pakutsotsa pace pokha azimbwezera, namcizitse konse.

20 Munthu akakantha mnyamata wace, kapena mdzakazi wace, ndi ndodo, ndipo akafa padzanja pace; ameneyo aliridwe ndithu.

21 Koma akakhala wosafa tsiku limodzi kapena awiri, asalirike, pakuti ndiye ndalama ya mbuye wace.

22 Akayambana amuna, nakakantha mkazi ali ndi pakati, kotero kuti abala, koma alibe kuphwetekwa; alipe ndithu, monga momwe amchulira mwamuna wa mkaziyo; apereke monga anena oweruza.

23 Koma ngati kuphweteka kukalipo, uzipereka moyo kulipa moyo,

24 diso kulipa diso, dzino kulipa dzino, dzanja kulipa dzanja, phazi kulipa phazi,

25 kutentha kulipa kutentha, bala kulipa bala, mkwapulo kulipa mkwapulo.

26 Munthu akampanda mnyamata wace, kapena mdzakazi wace, padiso, nalithudzula, azimlola amuke waufulu cifukwa ca diso lace.

27 Ndipo akagurula dzino la mnyamata wace, kapena dzino la mdzakazi wace, azimlola amuke waufulu cifukwa ca dzino lace.

28 Ng'ombe ikatunga mwamuna kapena mkazi, nafa, aiponyetu miyala ng'ombeyo, osadya nyama yace; koma mwini ng'ombeyo azimasuka.

29 Koma ngati ng'ombe ikatunga masiku adapitawo, ndipo anamcenjeza mwiniyo, koma osaisunga iye, ndipo ikapha mwamuna kapena mkazi, aiponye miyala ng'ombeyo, ndi mwini waceyo amuphenso.

30 Akamuikira dipo, azipereka ciombolo ca moyo wace monga mwa zonse adamuikira.

31 Ingakhale yatunga mwana wamwamuna kapena wamkazi, aicitire monga mwa ciweruzo ici.

32 Ng'ombeyo ikatunga mnyamata kapena mdzakazi, azipatsa mbuye wace ndalama za masekele a siliva makumi atatu, ndipo ng'ombeyo aiponye miyala.

33 Munthu akafukula dzenje, kapena akakumba dzenje, osalibvundikira, ndipo ikagwamo ng'ombe kapena buru,

34 mwini dzenje azilipa; azilipa ndalama kwa mwini nyamayo, koma yakufayo ndi yace.

35 Ng'ombe ya mwini ikapweteka ng'ombe ya mnzace, nifa, azigulitsa ng'ombe yamoyoyo, nagawe ndalama zace; naigawe, ndi yakufa yomweyo.

36 Kapena kudadziwika kuti ng'ombeyo ikatunga masiku adapitawo, koma osaisunga mwiniyo, azilipa ndithu, ng'ombe kulipa ng'ombe, koma yakufayo ndi yace.

22

1 Munthu akaba ng'ombe, kapena nkhosa, nakaipha, kapena kuigulitsa, azilipa ng'ombe zisanu pa ng'ombeyo; ndi nkhosa zinai pa nkhosayo,

2 Akampeza wakuba alimkuboola, nakamkantha kotero kuti wafa, palibe camwazi.

3 Litamturukira dzuwa, pali camwazi; wakubayo azilipa ndithu; ngati alibe kanthu, amgulitse pa umbala wace.

4 Akacipeza cakubaco ciri m'dzanja lace camoyo, ngakhale ng'ombe, kapena buru, kapena nkhosa, alipe mowirikiza.

5 Munthu akadyetsa coweta pabusa kapena pa munda wamphesa, atamasula coweta cace, ndipo citadya podyetsa pa mwini wace; alipe podyetsa pace poposa, ndi munda wa mphesa wace woposa.

6 Ukayaka moto, nukalandira kuminga, kotero kuti unyeketsa mulu wa tirigu, kapena tirigu wosasenga, kapena munda; woyatsa motoyo alipe ndithu.

7 Munthu akaikiza ndalama kapena cuma kwa mnansi wace, ndipo zibeka m'nyumba ya munthuyo; akapeza mbala, ilipe cowirikiza.

8 Akapanda kumpeza mbalayo, abwere naye mwini nyumbayo kwa oweruza, kumuyesa ngati anaika dzanja lace pa cuma ca mnansi wace.

9 Mlandu uti wonse wa colakwa, kunena za ng'ombe, za buru, za nkhosa, za cobvala, za kanthu kali konse kotayika, munthu anenako kali kace; mlandu wa onse awiri ufike kwa oweruza; iye amene oweruza amtsutsa alipe cowirikiza kwa mnansi wace.

10 Munthu akaikiza buru, kapena ng'ombe, kapena nkhosa, kapena coweta cina kwa mnansi wace, ndipo cikafa, kapena ciphwetekwa, kapena wina acipitikitsa osaciona munthu;

11 lumbiro la Yehova likhale pakati pa iwo awiri, kuti sanaturutsa dzanja lace pa cuma ca mnansi wace; ndipo mwiniyo azibvomereza, ndipo asalipe.

12 Koma ngati cidabedwa kwaoko ndithu, alipe kwa mwiniyo.

13 Ngati cajiwa ndithu, abwere naco cikhale mboni; asalipe pa cojiwaco.

14 Munthu akabwereka cinthu kwa mnansi wace, ndipo ciphwetekwa, kapena cifa, mwiniyo palibe, azilipa ndithu.

15 Akakhalapo mwiniyo, asalipe; ngati cagwirira nchito yakulipira, cadzera kulipira kwace.

16 Munthu akanyenga namwali wosapalidwa ubwenzi, nakagona nave, alipetu kuti akhale mkazi wace.

17 Atate wace akakana konse kumpatsa iye, alipe ndalama monga mwa colipa ca anamwali.

18 Wanyanga usamlola akhale ndi moyo.

19 Ali yense agona ndi coweta aphedwe ndithu.

20 Wakuphera nsembe mulungu wina, wosati Yehova yekha, aonongeke konse.

21 Ndipo usasautsa mlendo kapena kumpsinja; pakuti munali alendo m'dziko la Aigupto.

22 Musazunza mkazi wamasiye, kapena mwana wamasiye ali yense.

23 Ukawazunza ndi kakuti konse, nakandilirira pang'ono ponse iwowa, ndidzamvadi kulira kwao;

24 ndi mkwiyo wanga idzayaka, ndipo ndidzapha inu ndi lupanga; ndipo akazi anu adzakhala amasiye, ndi ana anu omwe.

25 Ukakongoletsa ndalama anthu anga osauka okhala nanu, usamkhalira ngati wangongole; usamwerengera phindu.

26 Ukati ulandire cikole kaya cobvala ca mnansi wako, koma polowa dzuwa ucibwezere kwa iye;

27 popeza copfunda cace ndi ici cokha, ndico cobvala ca pathupi pace; azipfundira ciani pogona? Ndipo kudzakhala kuti akandipfuulira Ine, ndidzamva; pakuti Ine ndine wacisomo.

28 Usapeputsa oweruza, kapena kutemberera mkuru wa anthu a mtundu wako.

29 Usacedwa kuperekako zipatso zako zocuruka, ndi zothira zako. Woyamba wa ana ako amuna undipatse Ine.

30 Uzitero nazo ng'ombe zako, ndi nkhosa zako; masiku asanu ndi atatu akhale ndi amai wace; tsiku lacisanu ndi citatu uzimpereka kwa Ine.

31 Ndipo muzindikhalira Ine anthu opatulika; cifukwa cace musamadya nyama yojiwa kuthengo; itayireni agaru.

23

1 Usatola mbiri yopanda pace; usathandizana naye woipa ndi kukhala mboni yocititsa ciwawa.

2 Usatsata unyinji wa anthu kucita coipa; kapena usacita umboni kumlandu, ndi kupatukira kutsata unyinji ndi kukhotetsa mlandu;

3 kapena usakometsera munthu wosauka pa mlandu wace.

4 Ukakomana ndi ng'ombe kapena buru wa mdani wako zirimkusokera, uzimbwezera izo ndithu.

5 Ukaona buru wa munthuwakudana nawe alikugona pansi ndi katundu wace, ndipo ukadaleka kuthandiza, koma uzimthandiza ndithu.

6 Usakhotetsa mlandu wa mnzako waumphawi.

7 Uzikhala kutali ndi mlandu wonama; ndipo usapha munthu wosacimwa ndi wolungama; pakuti sindidzayesa wolungama munthu woipa.

8 Usalandira cokometsera mlandu; pakuti cokometsera mlandu cidetsa maso a openya, nicisanduliza mlandu wa olungama,

9 Usampsinia mlendo; pakuti mudziwa mtima wa mlendo popeza munali alendo m'dziko la Aigupto.

10 Ndipo uzibzala m'munda mwako zaka zisanu ndi cimodzi, ndi kututa zipatso zako;

11 koma caka cacisanu ndi ciwiri uuleke, ugone; kuti aumphawi a anthu a mtundu wako adyemo ndipo zotsalira iwowa zoweta za kubusa zizidye; momwemo uzicita ndi munda wako wamphesa, ndimundawakowaazitona.

12 Uzicita nchito yako masiku asanu ndi limodzi, koma tsiku lacisanu ndi ciwiri uzipumula; kuti ng'ombe yako ndi buru wako zipumule, ndi kuti mwana wa mdzakaziwako ndi mlendo atsitsimuke.

13 Ndipo samalirani zonse ndanena ndi inu; nimusachule dzina la milungu yina; lisamveke pakamwa pako.

14 Muzindicitira loe madyerero katatu m'caka.

15 Uzisunga madyerero a mkate wopanda cotupitsa; masiku asanu ndi awiri uzidya mkate wopanda cotupitsa, monga ndinakuuza, nyengo yoikika, mwezi wa Abibu, pakuti m'menemo unaturuka m'Aigupto; koma asaoneke munthu pamaso panga opanda kanthu;

16 ndi madyerero a masika, zipatso zoyamba za nchito zako, zimene udazibzala m'munda; ndi madyerero a kututa, pakutha caka, pamene ututa nchito zako za m'munda.

17 Katatu m'caka amuna onse azioneka pamaso pa Ambuye Yehova.

18 Usapereka mwazi wa nsembe yanga pamodzi ndi mkate wacotupitsa; ndi mafuta a madyerero anga asagonamo kufikira m'mawa.

19 Uzibweca nazo zoyambayamba za m'munda mwako ku nyumba ya Yehova Mulungu wako. Usaphike mwana wa mbuzi mu mkaka wa mace. Mulungu aloniezana nao za Kanani.

20 Taona, ndituma mthenga akutsogolere, kukusunga panjira, ndi kukufikitsa pamalo pomwe ndakonzeratu.

21 Musamalire iye, ndi kumvera mau ace; musamwawitsa mtima, pakuti sadzakhululukira zoo lakwa zanu; popeza dzina langa liri m'mtima mwace.

22 Pakuti ukamveratu mau ace, ndi kucita zonse ndizilankhula, ndidzakhala mdani wa adani ako, ndipo ndidzasautsa akusautsa iwe.

23 Pakuti mthenga wanga adzakutsogolera, nadzakufikitsa kwa Aamori, ndi Ahiti, ndi Aperizi, ndi Akanani, Ahivi, ndi Ayebusi; ndipo ndidzawaononga.

24 Usagwadira milungu yao, kapena kuwatumikira, kapena kucita monga mwa nchito zao; koma uwapasule konse, ndi kugamulatu zoimiritsa zao.

25 Ndipo muzitumikira Yehova Mulungu wanu, potero adzadalitsa cakudya cako, ndi madzi ako; ndipo ndidzacotsa nthenda pakati pa iwe.

26 M'dziko mwanu simudzakhala wakutaya mwana, kapena wosabala; ndidzakwaniritsa kuwerenga kwa masiku ako.

27 Ndidzatumiza kuopsa kwanga kukutsogolere, ndipo ndidzapitikitsa anthu onse amene udzafika kwao, ndipo ndidzacita kuti adani ako onse adzakuonetsa m'mbuyo mwao.

28 Ndipo ndidzatumiza mabvu akutsogolere amene adzaingitsa Ahivi, Akanani, ndi Ahiti, pamaso pako.

29 Sindidzawaingista pamaso pako caka cimodzi; kuti dziko lingakhale bwinja, ndi zirombo za kuthengo zingakucurukire.

30 Ndidzawaingitsa pang'ono pang'ono pamaso pako, kufikira utacuruka, ndi kulandira dziko colowa cako.

31 Ndipo ndidzalemba malire ako kuyambira ku Nyanja Yofiira, kufikira ku nyanja ya Afilisiti, ndi kuyambira kucipululu kufikira ku Nyanja; popeza ndidzapereka okhala m'dzikolo m'dzanja lako, ndipo uziwaingitsa pamaso pako.

32 Usapangana nao, kapena ndi milungu yao.

33 Asakhale m'dziko lako iwowa, kuti angakulakwitse pa loe; pakuti ukatumikira milungu yao, kudzakukhalira msampha ndithu.

24

1 Ndipo iye ananena ndi Mose, Ukwere kudza kwa Yehova, iwe ndi Aroni, Nadabu ndi Abihu, ndi akuru a Israyeli makumi asanu ndi awiri; ndipo mugwadire pakudza kutali;

2 ndipo Mose yekha ayandikire kwa Yehova; koma asayandikire iwowa; ndi anthunso asakwere naye.

3 Ndipo Mose anadza nafotokozera anthu mau onse a Yehova, ndi masveruzo onse; ndipo anthu onse anabvomera pamodzi, nati, Mau onse walankhula Yehova tidzacita.

4 Ndipo Mose analembera mau onse a Yehova, nalawira kuuka mamawa, namanga guwa la nsembe patsinde pa phiri, ndi zoimiritsa khumi ndi ziwiri, kwa mafuko khumi ndi awiri a Israyeli.

5 Ndipo anatuma ana a Israyeli a misinkhu ya anyamata, ndiwo anapereka nsembe zopsereza, naphera Yehova nsembe zamtendere, zang'ombe.

6 Ndipo Mose anagawa mwaziwo, nathira wina m'zotengera, nawaza wina pa guwa la nsembe.

7 Ndipo anatenga buku la Cipangano, nawerenga m'makutu a anthu; ndipo iwo anati, Zonse zimene Yehova walankhula tidzacita, ndi kumvera.

8 Ndipo Mose anatenga mwaziwo, nawaza pa anthu, nati, Taonani mwazi wa cipangano, cimene Yehova anacita nanu, kunena za mau awa onse,

9 Ndipo Mose ndi Aroni, Nadabu ndi Abihu, ndi akuru a Israyeli makumi asanu ndi awiri anakwerako;

10 ndipo anapenya Mulungu wa Israyeli; ndipo pansi pa mapazi ace panali ngati mayalidwe oyera a miyala yasafiri, ndi ngati thupi la thambo loti mbe.

11 Koma sanaturutsa dzanja lace pa akuru a ena a Israyeli; ndipo anapenya Mulungu, nadya, namwa.

12 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Ukwere kudza kwa Ine m'phiri muno, nukhale pompano; ndipo ndidzakupatsa magome amiyala, ndi cilamulo ndi malamulo, ndawalembera kuti uwalangize.

13 Ndipo anauka Mose, ndi Yoswa mtumiki wace; ndipo Mose anakwera m'phiri la Mulungu.

14 Ndipo anati kwa akuru, Tilindeni kuno kufikira tidzabwera kwa inu; ndipo taonani, Aroni ndi Huri ali nanu; munthu akakhala ndi mlandu abwere kwa iwowa.

15 Ndipo Mose anakwera m'phirimo, ndi mtambo unaphimba phirilo,

16 Ndipo ulemerero wa Yehova unakhalabe pa phiri la Sinai, ndi mtambo unaliphimba masiku asanu ndi limodzi; ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri iye ali m'kati mwa mtambo anaitana Mose.

17 Ndipo maonekedwe a ulemerero wa Yehova anali ngati mota wonyeketsa pamwamba pa phiri, pamaso pa ana a Israyeli.

18 Ndipo Mose analowa m'kati mwa mtambo, nakwera m'phirimo; ndipo Mose anakhala m'phiri masiku makumi anai usana ndi usiku.

25

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2 Lankhula ndi ana a Israyeli, kuti anditengere copereka; ulandire copereka canga kwa munthu ali yense mtima wace umfunitsa mwini.

3 Ndipo coperekaco ucilandire kwa iwo ndi ici: golidi, ndi, siliva, ndi mkuwa,

4 ndi lamadzi, ndi: lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi;

5 ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wasitimu;

6 mafuta akuunikira, zonunkhira za mafuta odzoza, ndi za cofukiza ca pfungo lokoma;

7 miyala yaberulo, ndi miyala yoika paefodi, ndi pacapacifuwa.

8 Ndipo andimangire malo opatulika; kuti ndikhale pakati pao,

9 Monga mwa zonse Ine ndirikuonetsa iwe, cifaniziro ca kacisi, ndi cifaniziro ca zipangizo zace zonse, momwemo ucimange.

10 Ndipo azipanga likasa la mtengo wasitimu: utali wace mikono iwiri ndi hafu, kupingasa kwace mkono ndi hafu, msinkhu wace mkono ndi hafu.

11 Ndipo ulikute ndi golidi woona, ulikute m'kati ndi kubwalo, nulipangire mkombero wagolidi pozungulira pace.

12 Ndipo uliyengere mphete zinai zagolidi, ndi kuziika ku miyendo yace inai; mphete ziwiri pa mbali yace yina, ndi mphete ziwiri pa yina.

13 Ndipo uzipanga mphiko za mtengo wasitimu, ndi kuzikuta ndi golidi.

14 Nupise mphiko m'mphetezo pa mbali zace za likasa, zakunyamulira nazo likasalo.

15 Mphiko zikhale m'zimphete za likasa; asazisolole.

16 Ndipo uziika m'likasamo mboni imene ndidzakupatsa.

17 Ndipo uzipanga cotetezerapo ca golidi woona; utali wace mikono iwiri ndi hafu, ndi kupingasa kwace mkono ndi hafu.

18 Uzipanganso akerubi awiri agolidi; uwasule mapangidwe ace, pa mathungo ace awiri a cotetezerapo.

19 Nupange kerubi mmodzi ku thungo lino, ndi kerubi wina ku thungo lina; upange akerubi ocokera kucotetezerapo, pa mathungo ace awiri.

20 Ndipo akerubi afunyululire mapiko ao m'mwamba, ndi kuphimba cotetezerapo ndi mapiko ao, ndi nkhope zao zipenyane; nkhope za akerubi ziphenye kucotetezerapo,

21 Ndipo uziika cotetezerapo pamwamba pa likasa, ndi kuikamo mboni ndidzakupatsayo m'likasamo.

22 Ndipo pomwepo ndidzakomana ndi iwe, ow kulankhula ndi iwe, ndiri pamwamba pa cotetezerapo, pakati pa akerubi awiriwo okhala pa likasa la mboni, zonse zimene ndidzakuuza za ana a Israyeli.

23 Ndipo uzipanga gome la mtengo wasitimu; utali wace mikono iwiri, ndi kupingasa kwace mkono umodzi, ow msinkhu wace mkono ndi hafu.

24 Ndipo ulikute ndi golidi woona ndi kulipangira mkombero wagolidi pozungulira pace.

25 Nulipangire mitanda pozungulirapo yoyesa cikhato m'kupingasa kwace, ndi pamitanda pace pozungulira upangirepo mkombero wagolidi.

26 Nulipangire mphete zinai zagolidi, ndi kuika mphetezo pa ngondya zinai zokhala pa miyendo yace inai.

27 Mphetezo zikhale pafupi pa mitanda, zikhale zopisamo mphiko za kunyamulira nazo gome.

28 Ndipo uzipanga mphiko za mtengo wasitimu, ndi kuzikuta ndi golidi, kuti anyamulire nazo gome.

29 Ndipo uzipanga mbale zace, ndi zipande zace, ndi mitsuko yace, ndi zikho zace zakuthira nazo; uzipanga za golidi woona.

30 Ndipo uziikamkate woonekera pa gomelo pamaso panga nthawi zonse.

31 Ndipo uzipanga coikapo nyali ca golidi woona; coikapoco cisulidwe mapangidwe ace, tsinde lace ow thupi lace; zikho zace, mitu yace, ndi maluwa ace zikhale zocokera m'mwemo;

32 ndipo m'mbali zace muturuke mphanda zisanu ndi imodzi; mphanda zitatu za coikapo nyalico zituruke m'mbali yace yina, ndi mphanda zitatu za coikapo nyalico zituruke m'mbali inzace.

33 Ku mphanda yina kukhale zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi luwa; ndi ku mphanda inzace zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi luwa; zitere mphanda zisanu ndi imodzi zoturuka m'coikapo nyalico.

34 Ndipo pa coikapo nyali comwe pakhale zikho zinai zopangika ngati katungurume, mitu yace ndi maluwa ace;

35 pakhale mutu pansi pa mphaada ziwiri zoturuka m'mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri zoturuka m'mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri zoturuka m'mwemo; itere ku mphanda zisanu ndi imodzi zoturuka m'coikapo nyalico.

36 Mitu yao ndi mphanda zao zikhale zoturuka m'mwemo; conseci cikhale cosulika cimodzi ca golidi woona.

37 Ndipo uzipanga nyali zace, zisanu ndi ziwiri; ndipo ayatse nyali zace, ziwale pandunji pace.

38 Ndipo mbano zace, ndi zoolera zace, zikhale za golidi woona.

39 Acipange ici ndi zipangizo izi zonse za talente wa golidi woona.

40 Ndipo uyang'anire uzipanga monga mwacifaniziro cao, cimene anakuonetsa m'phirimo.

26

1 Ndipo uzipanga kacisi ndi nsaru zophimba khumi, za bafuta wa thonje losansitsa, ndi thonje lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira; uombemo akerubi, nchito ya mmisiri.

2 Utali wace wa nsaru yophimba imodzi ndiwo mikono makumi awiri kudza isanu ndi itatu, ndi kupingasa kwa nsaru imodzi ndiko mikono inai; nsaru zonse zikhale za muyeso umodzi.

3 Nsaru zisanu zilumikizane yina ndi inzace; ndi nsaru zisanu zina zilumikizane yina ndi inzace.

4 Ndipo uziika magango a nsaru yamadzi m'mphepete mwace mwa nsaru imodzi, ku mkawo wa cilumikizano; nucite momwemo m'mphepete mwace mwa nsaru ya kuthungoya cilumikizano dna.

5 Uziika magango makumi asanu pa nsaru yocingira imodzi, nuikenso magango makumi asanu m'mphepete mwace mwa nsaru ya cilumikizano cina; ndipo magango akomanizane lina ndi linzace.

6 Uzipanganso zokowera makumi asanu zagolidi, ndi kumanga nsaruzo pamodzi ndi zokowerazo; kuti kacisi akhale mmodzi.

7 Ndipo uziomba nsaru zophimba za ubweya wa mbuzi zikhale hema pamwamba pa kacisi; uziomba nsaru khumi ndi imodzi.

8 Utali wace wa nsaru imodzi ndiwo mikono makumi atatu, ndi kupingasa kwace kwa nsaru imodzi ndiko mikono inai; nsarukhumi ndi imodzi zikhale za muyeso womwewo.

9 Nuzisoka pamodzi nsaru zisanu pa zokha ndi nsaru zisanu ndi imodzi pa zokha, nupinde nsaru yacisanu ndi cimodziyo pa khomo la hema.

10 Ndipo uziika magango makumi asanu m'mphepete mwa nsaru imodzi, ya kuthungo ya cilumikizano, ndi magango makumi asanu m'mphepete mwa nsaru ya kuthungo ya cilumikizano cina.

11 Ndipo uzipanga zokowera makumi asanu zamkuwa, ndi kukowetsa zokowerazo m'magangomo, ndi kumanga pamodzi hemalo likhale limodzi.

12 Ndipo cotsalaco pa nsaru za hemalo, hafu yace ya nsaru yotsalirayo, icinge pambuyo pace pa kacisi.

13 Ndi mkono wa pa mbali yino, ndi mkono wa pa mbali inzace, wakutsalira m'utali wace wa nsaru za hemalo, icinge pambali zace za kacisi, mbali yino ndi mbali yina, kumphimba.

14 Ndipo uzipangira hema cophimba ca zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi cophimba za zikopa za akatumbu pamwamba pace.

15 Ndipo uzipangira kacisi matabwa oimirika, a mtengo wasitimu.

16 Utali wace wa thabwa limodzi ndiwo mikono khumi, ndi kupingasa kwace kwa thabwali mkono ndi hafu.

17 Pa thabwa limodzi pakhale mitsukwa iwiri, yomangika pamodzi; uzitero pa matabwa onse a kacisi.

18 Ndipo uzipanga matabwa a kacisi, matabwa makumi awiri ku mbali ya kumwela, kumwela.

19 Nuzipanga makamwa makumi anai asiliva pansi pa matabwa makumi awiri; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi kwa mitsukwa yace iwiri, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina kwa mitsukwa yace iwiri;

20 ndi pa mbali yace yina ya kacisi, mbali ya kumpoto, pakhale matabwa makumi awiri; ndi makamwa asiliva makumi anai;

21 makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina.

22 Ndipo uzipanga matabwa asanu ndi limodzi kwa mbali ya kacisi ya kumbuyo kumadzulo.

23 Nupange matabwa awiri a ngondya za kacisi za kumbuyo.

24 Ndipo akhale ophatikizika pamodzi patsinde, nakhalenso ophatikizika pamodzi kumutu kwace ndi mphete imodzi; azitero onse awiri; azikhala a ngondya ziwiri.

25 Ndipo pakhale matabwa asanu ndi atatu, ndi makamwa ao asiliva, ndiwo makamwa khumi mphambu asanu ndi limodzi; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina.

26 Ndipo uzipanga mitanda ya mtengo wasitimu; isanu ya matabwa a pa mbali yina ya kacisi,

27 ndi mitanda isanu ya matabwa a Pel mbali yina ya kacisi, ndi mitanda isanu ya matabwa a pa mbali ya kacisi ya kumbuyo kumadzulo.

28 Ndi mtanda wa pakati pa matabwa ufikire kuthungo.

29 Ndipo uzikuta matabwa ndi golidi, ndi kupanga mphete zao zagolidi zopisamo mitandayo; uzikutanso mitandayo ndi golidi.

30 Ndipo uutse kacisi monga mwa makhalidwe ace amene anakusonyeza m'phiri.

31 Ndipo uziomba nsaru yocinga ya thonje lamadzi, ndi lofiirira ndi lofiira, ndi la bafuta wa thonje losansitsa, aiombe ndi akerubi nchito ya mmisiri;

32 ndipo uicinge pa mizati inai ya mitengo wasitimu, zokuta ndi golidi; zokowera zao zikhale zagolidi, ndi makamwa anai asiliva.

33 Ndipo uzicinga nsaru yocinga pa zokowerazo, nulowetse likasa la mboni kukati kwa nsaru yocinga; ndipo nsaru yocingayo idzakugawirani pakati pa malo opatulika ndi malo opatulikitsa.

34 Ndipo uziika cotetezerapo pa likasa la mboni, m'malo opatulikitsa.

35 Nuziika gomelo kunja kwa nsaru yocinga, ndi coikapo nyali pandunji pa gome, pa mbali ya kumwela ya kacisi; koma uike gomelo pa mbali ya kumpoto,

36 Ndipo uziomba nsaru yotsekera pa khomo la bema, ya lakuda, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, nchito ya wopikula.

37 Ndipo uzipangira nsaru yotsekerayo nsanamira zisanu za mtengo wasitimu, ndi kuzikuta ndi golidi; zokowera zao zikhale zagolidi; nuziyengera makamwa asanu amkuwa.

27

1 Ndipo upange guwa la nsembe la mtengo wasitimu, utali wace mikono isanu, ndi kupingasa kwace mikono isanu, guwa la nsembelo likhale lampwamphwa, ndi msinkhu wace mikono itatu.

2 Ndipo uzipanga nyanga zace pa ngondya zace zinai; nyanga zace zikhale zoturuka m'mwemo: nulikute ndi mkuwa:

3 Ndipo uzipanga zotayira zace zakulandira mapulusa ace, ndi zoolera zace, ndi mbale zowazira zace, ndi mitungo yace, ndi zoparira moto zace; zipangizo zace zonse uzipanga zamkuwa.

4 Ndipo ulipangire made, malukidwe ace ndi amkuwa; nupange pa malukidwewo ngondya zace zinai mphete zinai zamkuwa.

5 Nuwaike pansi pa matso a guwa la nsembelo posungulira, kuti malukidwe alekeze pakati pa guwa la nsembelo.

6 Ndipo upangire guwa la nsembe mphiko, mphiko za mtengo wasitimu, ndi kuzikuta ndi mkuwa.

7 Ndipo apise mphiko m'mphetezo kuti mphikozo zikhale pa mbali ziwiri za guwa la nsembe polinyamula.

8 Ulipange lagweregwere ndi matabwa; monga anakuonetsa m'phirimo; alipange momwemo.

9 Upangenso bwalo la cihema; pa mbali yace ya kumwela, kumwela, pakhale nsaru zocingira zakubwaloza nsaru ya bafuta wa thonje losansitsa, utali wace wa pa mbali imodzi mikono zana;

10 ndi nsici zace makumi awiri, ndi makamwa ao makumi awiri akhale amkuwa; zokowera za nsici ndi mitanda yace zikhale zasiliva.

11 Momwemonso pa mbali ya kumpoto m'utali mwace pakhale nsaru zocingira za mikono zana limodzi m'utali mwace; ndi nsici zace makumi awiri, ndi makamwa ao akhale amkuwa; zokowera za nsicizo ndi mitanda yace zikhale zasiliva.

12 Ndipo m'kupingasa kwa bwaloli pa mbali ya kumadzulo mukhale nsaru zocingira za mikono makumi asanu; nsici zace zikhale khumi, ndi makamwa ao khumi.

13 Ndipo m'kupingasa kwace kwa bwalo pa mbali ya kum'mawa, kum'mawa, mukhale mikono makumi asanu.

14 Ndi nsaru zocingira za pa mbali imodzi ya kucipata zikhale za mikono khumi ndi isanu; nsici zace zikhale zitatu, ndi makamwa ao atatu.

15 Ndi pa mbali yina pakhale nsaru zocingira za mikono khumi ndi isanu; nsici zace zikhale zitatu, ndi makamwa ao atatu.

16 Ndipo pa cipata ca bwalolo pakhale nsaru yotsekera ya mikono makumi awiri, ya lamadzi ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, nchito ya wopikula; nsici zace zikhale zinai, ndi makamwa ao anai.

17 Nsici zonse za pabwalo pozungulira zimangike pamodzi ndi mitanda yasiliva; zokowera zao zasiliva, ndi makamwa ao amkuwa.

18 Utali wace wa bwalolo ukhale wa mikono zana limodzi, ndi kupingasa kwace makumi asanu monsemo, ndi msinkhu wace wa mpanda mikono isanu; ukhale wabafuta wa thonje losansitsa; ndi makamwa a nsicizo akhale amkuwa.

19 Zipangizo zonse za kacisi, m'macitidwe ace onse, ndi ziciri zace zonse, ndi ziciri zonse za bwalo lace, zikhale zamkuwa.

20 Ndipo uuze ana a Israyeli akutengere mafuta a azitona oyera opera akuunikira, kuti awalitse nyali kosalekeza.

21 Aroni ndi ana ace aikonze m'cihema cokomanako, kunja kwa nsaru yocinga yokhala kumboni, kuyambira madzulo kufikira m'mawa; likhale lemba losatha mwa mibadwo yao, alisunge ana a Israyeli.

28

1 Ndipo akuyandikire Aroni mbale wako, ndi ana ace amuna pamodzi naye, mwa ana a Israyeli, kuti andicitire Ine nchito ya nsembe, ndiwo Aroni, Nadabu, ndi Abihu, Eleazara ndi ltamara, ana a Aroni.

2 Ndipo usokere Aroni mbale wako zobvala zopatulika, zikhale zaulemerero ndi zokoma.

3 Ndipou lankhule ndi onse a mtima waluso, amene ndawadzaza ndi mzimu waluso, kuti amsokere Aroni zobvala apatulidwe nazo, andicitire Ine nchito ya nsembe.

4 Ndipo zobvala azisoka ndizi: capacifuwa ndi efodi, ndi mwinjiro, ndi malaya opikapika, ndi nduwira, ndi mpango; tero apangire Aroni mbale wako ndi ana ace zobvala zopatulika, kuti andicitire Ine nchito ya nsembe,

5 Ndipo atenge golidi, ndi lamadzi ndi lofiirira ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

6 Naombe efodi ndi golidi, ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira ndi bafuta wa thonje losansitsa, nchito ya mmisiri.

7 Akhale nazo zapamapewa ziwiri zomangika ku nsonga zace ziwiri, kuti amangike nazo.

8 Ndipo mpango wa efodi, wokhala pamenepo, kuti ammange nao, ukhale wa ciombedwe comweco, ndi woombera kumodzi, wagolidi, ndi thonje lamadzi, ndi lofiirira ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

9 Ndipo utenge miyala iwiri yaberulo, nulocepo maina a ana a Israyeli;

10 maina asanu ndi limodzi pa mwala wina, ndi maina asanu ndi limodzi otsala pa mwala unzace, mwa kubadwa kwao.

11 Uloce miyala iwiriyo ndi maina a ana a Israyeli, monga mwa nchito ya woloca miyala, monga malembedwe a cosindikizira, uipange igwirike ndi zoikamo zagolidi,

12 Ndipo ulike miyala iwiriyo pa zapamapewa za efodi, ikhale miyala ya cikumbutso ca ana a Israyeli; ndipo Aroni azinyamula maina ao pa mapewa ace awiri, akhale cikumbutso pamaso pa Yehova.

13 Ndipo upange zoikamo za golidi;

14 ndi maunyolo awiri a golidi woona; uwapote ngati zingwe, nchito yopota; numange maunyolo opotawo pazoikamo.

15 Upangenso capacifuwa ca ciweruzo, nchito ya mmisiri; uciombe mwa ciombedwe ca efodi; uciombe ndi golidi, lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

16 Cikhale campwamphwa, copindika, utali wace cikhato cimodzi, ndi kupingasa kwace cikhato cimodzi.

17 Ndipo uikepo miyala yoikikapo, mizere inai ya miyala; mzere wa odemu, pitida, ndi bareketi, ndiyo ya mzere woyamba;

18 ndi mzere waciwiri wa nofeki, safiri, ndi yahaloni;

19 ndi mizere wacitatu wa lesemu, sibu, ndi akalama;

20 ndi mzere wacinai wa tarisisi, sohamu, ndi yasefe; zikhale zogwirika ndi golidi m'zoikamo zao.

21 Ndi miyalayi ikhale monga mwa maina a ana a Israyeli, khumindiawiri, monga maina ao; monga malocedwe a cosindikizira, yonse ikhale monga maina ao, kwa mafuko khumi ndi awiri.

22 Upangenso maunyolo pa capacifuwa ngati zingwe, nchito yopota, ya golidi woona.

23 Nupangire pa capacifuwa mphete ziwiri zagolidi, ndi kuzika mphete ziwirizo pa nsonga zace ziwiri za capacifuwa.

24 Numange maunyolo awiri opota agolidi ku mphete ziwiri pansonga pace pa capacifuwa.

25 Koma nsonga zace ziwiri za maunyolo opotawo uzimange ku zoikamo ziwiri, ndi kuziika pa zapamapewa ziwiri za efodi, m'tsogolo mwace.

26 Ndipo upange mphete ziwiri zagolidi, ndi kuzimanga pa nsonga zace ziwiri za capacifuwa, m'mphepete mwace, m katimo ku mbali ya kuefodi.

27 Upangenso mphete ziwiri zagolidi, ndi kuzimanga pa zapamapewa ziwiri za efodi, m'munsi, ku mbali yace ya kutsogolo, pafupi pa msoko wace, pamwamba pa mpango wa efodi.

28 Ndipo amange capacifuwa pa mphete zace ndi mphete za efodi ndi mkuzi wamadzi, kuti cikhale pa mpango wa efodi; ndi kuti capacifuwa cisamasuke paefodi,

29 Ndipo Aroni azinyamula maina a ana a Israyeli pa capacifuwa ca ciweruzo pamtima pace, pakulowa iye m'malo opatulika, akhale cikumbutso pankhope pa Yehova kosalekeza.

30 Ndipo uike Urimu ndi Tumimu mwa capacifuwa ca ciweruzo; ndipo zikhale pa mtima wa Aroni, pakulowa iye pamaso pa Yehova; ndipo Aroni azinyamula ciweruzo ca ana a Israyeli pamtima pace pamaso pa Yehova kosalekeza.

31 Ndipo uombe mwinjiro wa efodi ndi lamadzi lokha.

32 Ndipo polowa mutu pakhale pakati pace; pakhale mkawo pozungulira polowa pace, wa nchito yoomba, ngati polowa pa malaya ociniiriza, pangang'ambike.

33 Ndipo pa mbinyiru wace upange makangaza a lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiirira, pambinyiru pace pozungulira, ndi kuwapakiza ndi miliu yagolidi pozungulira;

34 mliu wagolidi ndi khangaza, mliu wagolidi ndi khangaza, pa mbinyiru wa mwinjiro pozungulira.

35 Ndipo Aroni aubvale kuti atumikire nao; ndipo limveke liu lace pakulowa iye m'malo opatulika pamaso pa Yehova, ndi pakuturuka iye, kuti asafe.

36 Ndipo upange golidi waphanthiphanthi woona, ndi kulocapo, monga malocedwe a cosindikizira. KUPATULIKIRA YEHOVA.

37 Nuciike pamkuzi wamadzi, ndipo cikhale panduwira, cikhale patsogolo pace pa nduwira.

38 Ndipo cizikhala pamphumi pace pa Aroni, ndipo Aroni azinyamula mphulupulu ya zopatulidwa, zimene ana a Israyeli azipatulira, ndi zopereka zao zonse zopatulira; ndipo cizikhala pamphumi pace kosalekeza, kuti alandiridwe pamaso pa Yehova.

39 Ndipo upikule maraya am'kati abafuta a thonje losansitsa, nusoke nduwira wabafuta, nusokenso mpango wopikapika.

40 Ndipo usokere ana a Aroni maraya am'kati, nuwasokere mipango; uwasokerenso akapa akhale aulemerero ndi okoma.

41 Ndipo ubveke nazo Aroni mbale wako, ndi ana ace omwe; ndi a kuwadzoza, ndi kudzaza dzanja lao, ndi kuwapatula, andicitire Ine nchito ya nsembe.

42 Uwasokerenso zobvala za miyendo za bafuta wa thome losansitsa kubisa marisece ao; ziyambire m'cuuno zifikire kuncafu.

43 Ndipo azibvale Aroni, ndi ana ace, pakulowa iwo ku cihema cokomanako, kapena poyandikiza iwo ku guwa la nsembe kutumikira m'malo opatulika; anganyamule mphulupulu, nangafe; likhale lemba losatha la iye ndi mbumba zace pambuyo pace.

29

1 Ici ndico uwacitire kuwapatula, andicitire nchito ya nsembe: tenga ng'ombe yamphongo, ndi nkhosa ziwiri zamphongo zangwiro,

2 ndi mkate wopanda cotupitsa, ndi timitanda topanda cotupitsa tosanganiza ndi mafuta, ndi timitanda taphanthi topanda cotupitsa, todzoza ndi mafuta; utipange ndi ufa wosalala watirigu.

3 Ndipo uziike mu mtanga umodzi, ndi kubwera nazo mumtanga, pamodzi ndi ng'ombe yamphongo ndi nkhosa ziwiri zamphongo.

4 Ndipo ubwere nao Aroni ndi ana ace amuna ku khomo la cihema cokomanako indi kuwasambitsa m'madzi.

5 Pamenepo utenge zobvalazo ndi kubveka Aroni maraya am'kati, ndi mwinjiro wa efodi, ndi efodi, ndi capacifuwa, ndi kummangira m'cuuno ndi mpango wa efodi woluka mwanzeru;

6 ndipo uike nduwira pamutu pace, ndi kuika korona wopatulika panduwirapo.

7 Pamenepo utenge mafuta odzoza nao nuwatsanulire pamutu pace, ndi kumdzoza.

8 Ndipo ubwere nao ana ace amuna ndi kuwabveka maraya am'kati.

9 Uwamangirenso Aroni ndi ana ace amuna mipango m'cuuno mwao, nuwamangire akapa pamutu pao; ndipo akhale ansembe mwa lemba losatha; nudzaze dzanja la Aroni ndi dzanja la ana ace amuna,

10 Ndipo ubwere nayo ng'ombe yamphongo patsogolo pa cihema cokomanako; ndipo Aroni ndi ana ace amuna aike manja ao pamutu pa ng'ombe yamphongoyo.

11 Nuphe ng'ombe yamphongoyo pamaso pa Yehova, pa khomo la cihema cokomanako.

12 Pamenepo utapeko pa mwazi wa ng'ombe yamphongo, ndi kuupaka pa nyanga za guwa la nsembe ndi cala cako, nutsanulire mwazi wonse pa tsinde la guwa la nsembe.

13 Nutenge mafuta onse akukuta matumbo, ndi cokuta ca mphafa ndi imso ziwiri, ndi mafuta ali pa izo, ndi kuzitentha pa guwa la nsembe.

14 Koma nyama ya ng'ombeyo, ndi cikopa cace, ndi cipwidza cace, uzitentha izi ndi moto kunja kwa cigono; ndiyo nsembe yaucimo.

15 Utengenso nkhosa yamphongo imodziyo; ndi Aroni ndi ana ace amuna aike manja ao pamutu pa nkhosa yamphongoyo.

16 Nuiphe nkhosa yamphongoyo, ndi kutenga mwazi wace, ndi kuuwaza pa guwa la nsembe pozungulira.

17 Ndipo upadzule nkhosa yamphongo m'ziwalo zace, ndi kutsuka matumbo ace, ndi miyendo yace, ndi kuziika pa ziwalo zace, ndi pamutu pace.

18 Pamenepo upsereze, nkhosa yamphongo yonse pa guwa la nsembe; ndiyo nsembe yopsereza ya Yehova, ya pfungo lokoma; ndiyo nsembe yamoto ya Yehova.

19 Ndipo utenge nkhosa yamphongo yinayo; ndi Aroni ndi ana ace amuna aike manja ao pamutu pa nkhosa yamphongoyo.

20 Pamenepo uiphe nkhosa yamphongoyo, nutapeko pa mwazi wace, ndi kuupaka pa ndewerere ya khutu lamanja la Aroni, ndi pa ndewerere ya khutu lamanja la ana ace amuna, ndi pa cala cacikulu ca dzanja lao lamanja, ndi pa cala cacikulu ca phazi lao lamanja, ndi kuuwaza mwaziwo pa guwa la nsembe posungulira,

21 Ndipo utapeko pamwazi uli pa guwa la nsembe, ndi pa mafuta akudzoza nao, ndi kuwaza pa Aroni, ndi pa zobvala zace, ndi pa ana ace amuna, ndi pa zobvala za ana ace amuna, pamodzi ndi iye; kuti akhale wopatulidwa, ndi zobvala zace zomwe, ndi ana ace amuna ndi zobvala zao zomwe pamodzi ndi iye.

22 Utengenso mafuta a nkhosa yamphongoyo, ndi me ira, ndi mafuta akukuta mat umbo, ndi cokuta ca mphafa, ndi imso ziwiri, ndi mafuta ali pamenepo, ndi mwendo wam'mwamba wa ku dzanja lamanja; pakuti ndiyo nkhosa yamphongo ya kudzaza manja;

23 ndi mkate wamphumphu umodzi, ndi kamtanda ka mkate wosanganiza ndi mafuta, ndi kamtanda kamodzi kaphanthi, ziri mu mtanga wa mkate wopanda cotupitsa wokhala pamaso pa Yehova;

24 ndipo uike zonsezo m'manja a Aroni, ndi m'manja a ana ace amuna; nuziweyule nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.

25 Pamenepo uzilandire m'manja mwao, ndi kuzipsereza pa guwa la nsembe, pa nsembe yopsereza, zicite pfungo lokoma pamaso pa Yehova; ndiyo nsembe yamoto ya Yehova.

26 Ndipo utenge nganga ya nkhosa yamphongo yodzaza manja ya Aroni, ndi kuiweyula ikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ndipo ikhale gawo lako.

27 Ndipo upatule nganga va nsembe yoweyula, ndi mwendo wam'mwamba wa nsembe yokweza, imene anaiweyula, ndi imene anaikweza, za nkhosa yamphongo yakudzaza manja; ziri za Aroni, ndi za ana ace amuna;

28 ndipo zikhale za Aroni ndi za ana ace amuna, mwa lemba losatha, ziwadzere kwa ana a Israyeli; popeza ndiyo nsembe yokweza; ndipo ikhale nsembe yokweza yodzera kwa ana a Israyeli, ya kwa nsembe zamtendere zao, ndiyo nsembe yao yokweza ya Yehova.

29 Ndipo zobvala zopatulika za Aroni zikhale za ana ace amuna pambuyo pace, kuti awadzoze atazibvala, nadzaze manja ao atazibvala;

30 mwana wace wamwamuna amene adzakhala wansembe m'malo mwace azibvala masiku asanu ndi awiri, pakulowa iye m'cihema cokomanako kutumikira m'malo opatulika.

31 Ndipo utenge nkhosa yamphongo yodzaza manja, nuphike nayama yace m'malo opatulika.

32 Ndipo Aroni ndi ana ace amuna adye nyama ya nkhosa yamphongoyo, ndi mkate uli mumtanga, pa khomo la cihema cokomanako.

33 Ndipo adye zimene anacita nazo coteteza, kuti awadzaze manja ndi kuwapatulitsa; koma mlendo asadyeko, pakuti nzopatulika izi.

34 Ndipo ikatsalako nyama yodzaza manja, kapena mkate kufikira m'mawa, pamenepo utenthe zotsalazo ndi moto; asazidye popeza ncopatulika ici.

35 Ndipo utero nao Aroni, ndi ana ace amuna, monga mwa zonse ndakuuza; udzaze manja ao masiku asanu ndi awiri.

36 Nukonze ng'ombe yamphongo, ndiyo nsembe yaucimo yakuteteza nayo, tsiku ndi tsiku; ndipo uyeretsa guwa la nsembe, pakucita coteteza pamenepo; ndipo ulidzoze kulipatula.

37 Ucitire guwa la nsembe coteteza masiku asanu ndi awiri ndi kulipatula; ndipo a guwa la nsembelo likhale lopatulikitsa; ciri conse cikhudza guwa la nsembelo cikhale copatulika.

38 Koma izi ndizo uzikonza pa guwa la nsembelo; ana a nkhosa awiri a caka cimodzi, tsiku ndi tsiku kosalekeza.

39 Mwana wa nkhosa wina ukonze m'mawa; ndi mwana wa nkhosa wina ukonze madzulo;

40 ndi pa mwana wa nkhosa mmodziyo pakhale limodzi la magawo khumi la ufa wosalala, wosanganiza ndi limodzi la magawo anai la hini wa mafuta opera; ndi limodzi la magawo anai la hini wa vinyo, likhale nsembe yothira.

41 Ndi mwana wa nkhosa wina ukonze madzulo; umkonze umo unacitira copereka ca m'mawa ndi nsembe yace yothira, akhale pfungo lokoma, nsembe yamoto ya Yehova.

42 Ikhale nsembe yopsereza yosalekeza ya mwa mibadwo yanu, pa khomo la cihema cokomanako, pamaso pa Yehova, kumene ndidzakomana nanu, kulankhula nawe komweko.

43 Ndipo pamenepo ndidzakomana ndi ana a Israyeli; ndipo cihema cidzapatulidwa ndi ulemerero wanga.

44 Ndipo ndidzapatula cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe; ndidzapatulanso Aroni ndi ana ace amuna omwe, andicitire nchito ya nsembe.

45 Ndipo ndidzakhala pakati pa ana a Israyeli, ndi kukhala Mulungu wao.

46 Ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wao, amene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto, kuti ndikhale pakati pao. Ine ndine Yehova Mulungu wao.

30

1 Ndipo upange guwa la nsembe la kufukizapo; ulipange la mtengo wasitimu.

2 Utali wace ukhale mkono, ndi kupingasa kwace mkono; likhale lampwamphwa; ndi msinkhu wace mikono iwiri; nyanga zace zituruke m'mwemo.

3 Ndipo ulikute ndi golidi woona, pamwamba pace ndi mbali zace zozungulira, ndi nyanga zace; ulipangirenso mkombero wagolidi pozungulira,

4 Ndipo ulipangire mphete ziwiri zagolidi pansi pa mkombero wace; uziike pa nthiti zace ziwiri, pa mbali zace ziwiri; zikhale zopisamo mphiko kulinyamula nazo.

5 Ndipo upange mphiko za mtengo wasitimu, ndi kuzikuta ndi golidi.

6 Nuliike cakuno ca nsaru yocinga iri ku likasa la mboni, patsogolo pa cotetezerapo ciri pamwamba pa mboni, pomwe ndidzakomana ndi iwe.

7 Ndipo Aroni azifukizapo cofukiza ca zonunkhira zokoma m'mawandim'mawa, pamene akonza nyalizo, acifukize.

8 Ndipo pamene Aroni ayatsa nyalizo madzulo, acifukize cofukiza cosatha pamaso pa Yehova mwa mibadwo yanu,

9 Musafukizapo cofukiza cacilendo, kapena nsembe yopsereza, kapena copereka; musathirepo nsembe yothira.

10 Ndipo Aroni azicita coteteza pa nyanga zace kamodzi m'caka; alicitire coteteza ndi mwazi wa nsembe yaucimo ya coteteza, mwa mibadwo yanu; ndilo lopatulikitsa la Yehova.

11 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

12 Pamene uwerenga ana a Israyeli, monga mwa mawerengedwe ao, munthu yense apereke kwa Yehova ciombolo ca pa moyo wace, pa kuwerengedwa iwowa; kuti pasakhale mliri pakati pao, pakuwerengedwa iwowa.

13 Ici acipereke, yense wakupita kwa owerengedwa; limodzi la magawo awiri a sekeli, monga sekeli la malo opatulika; (sekeli ndilo magera makumi awiri) limodzi la magawo awiri a sekeli, ndilo copereka ca Yehova.

14 Yense wakupita kwa owerengedwawo, wa zaka makumi awiri ndi wa mphambu zace, apereke coperekaco kwa Yehova.

15 Wacuma asacurukitsepo, ndi osauka asacepse pa limodzi mwa magawo awiri a sekeli, pakupereka copereka kwa Yehova, kucita coteteza ca miyoyo yanu.

16 Ndipo uzilandira ndarama za coteteza kwa ana a Israyeli, ndi kuzipereka pa nchito ya cihema cokomanako; kuti zikhale cikumbutso ca ana a Israyeli pamaso pa Yehova, kucita coteteza ca miyoyo yanu.

17 Ndipo Yehova analankhula ndi Mose, ndi kuti,

18 Upangenso mkhate wamkuwa, ndi tsinde lace lamkuwa, wakusambiramo; nuuike pakati pa ciliema cokomanako ndi guwa la nsembe, ndi kuthiramo madzi.

19 Ndipo Aroni ndi ana ace amuna azisambiramo manja ao ndi mapazi ao;

20 pakulowa iwo m'cihema cokomanako asambe ndi madzi, kuti angafe; kapena poyandikiza guwa la nsembe kutumikirako, kufukiza nsembe yamoto ya Yehova;

21 asambe manja ao ndi mapazi ao, kuti angafe: liwakhalire lemba losatha, kwa iye ndi kwa mbeu zace, mwa mibadwo yao.

22 Yehova ananenanso ndi Mose, ndi kuti,

23 Udzitengerenso zonunkhira zomveka, mure woyenda masekeli mazana asanu, ndi kinimani lonunkhira limodzi mwa magawo awiri a mureyo, ndilo masekeli mazana awiri kudza makumi asanu, ndi kane lonunkhira mazana awiri kudza makumi asanu,

24 ndi kida mazana asanu, monga sekeli la malo opatulika, ndi mafuta a azitona hini limodzi;

25 ndipo ukonze nazo mafuta odzoza opatulika, osanganizika monga mwa macitidwe a wosanganiza; akhale mafuta odzoza opatulika.

26 Ndipo udzoze nao cihema cokomanako, ndi likasa la mboni,

27 ndi gomelo ndi zipangizo zace zonse, ndi coikapo nyali ndi zipangizo zace,

28 ndi guwa la nsembe lofukizapo, ndi guwa la nsembe yopsereza ndi zipangizo zace zonse, ndi mkhate wosambiramo ndi tsinde lace.

29 Ndipo uzipatule, kuti zikhale zopatulika ndithu; zonse zakuzikhudza zidzakhala zopatulika.

30 Ndipo udzoze Aroni ndi ana ace amuna, ndi kuwapatula andicitire nchito ya nsembe.

31 Nulankhule ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Awa ndi mafuta odzoza opatulika a Ine mwa mibadwo yanu.

32 Asawatsanulire pa thupi la munthu; kapena musakonza ena onga awa, mwa makonzedwe ace; awa ndiwo opatulika, muwayese opatulika.

33 Ali yense amene akonza ena otere, kapena ali yense awaika pa mlendo, ameneyo asazidwe kwa anthu a mtundu wace.

34 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Udzitengere zonunkhira, natafi, ndi sekeleti, ndi kelebuna; zonunkhira pamodzi ndi libano loona; miyeso yofanana;

35 ndipo uzikonza nazo cofukiza, cosanganiza mwa macitidwe a wosanganiza, cokometsera ndi mcere, coona, copatulika;

36 nupere cina cisalale, nuciike cakuno ca mboni m'cihema cokomanako, kumene ndidzakomana ndi iwe; uciyese copatulika ndithu.

37 Koma za cofukizaco ucikonze, musadzikonzere nokha cina, mwa makonzedwe ace amene; muciyese copatulika ca Yehova.

38 Ali yense wokonza cina cotere kununkhizapo, asadzidwe kwa anthu a mtundu wace.

31

1 Za amisiri opanga nchitoyi, Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2 Taona ndaitana ndi kumchula dzina lace, Bezaleli, mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa pfuke la Yuda;

3 ndipo ndamdzaza nd mzimu wa Mulungu, ndi luso, ndi nzeru, ndi cidziwitso, ndi m'nchito ziri zonse,

4 kulingirira nchito zaluso, kucita ndi golidi ndi siliva ndi mkuwa,

5 ndi kuzokota miyala yoikika, ndi kuzokota mtengo, kucita nchito ziri zonse.

6 Ndipo Ine, taona, ndampatsa Aholiabu, mwana wa Ahisama, wa pfuko la Dani, akhale naye; ndipo ndaika luso m'mitima ya onse a mtima waluso, kuti apange zonse ndakuuza iwe;

7 cihema cokomanako, likasa la mboni, ndi cotetezerapo ciri pamwamba pace, ndi zipangizo zonse za cihemaco;

8 ndi gomelo ndi zipangizo zace, ndi coikapo nyali coona ndi zipangizo zace, ndi guwa la nsembe lofukizapo;

9 ndi guwa la nsembe yopsereza ndi zipangizo zace zonse, ndi mkhate ndi tsinde lace;

10 ndi zobvala zotumikira nazo, ndi zobvala zopatulika za Aroni wansembe, ndi zobvala za ana ace, zakucita nazo nchito ya nsembe;

11 ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca zonunkhira zokoma za malo opatulika; azicita monga mwa zonse ndakuuza iwe.

12 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

13 Koma iwe, lankhula ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Muzisunga masabata anga ndithu; pakuti ndiwo cizindikilo pakati pa Ine ndi inu mwa mibadwo yanu; kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova wakukupatulani.

14 Ndipo muzisunga Sabata; popeza ndilo lopatulika la kwa inu; ali yense wakuliipsa aphedwe ndithu; pakuti ali yense wakugwira nchito m'mwemo, munthu ameneyo asadzidwe mwa anthu a mtundu wace.

15 Agwire nchito masiku asanu ndi limodzi; koma lacisanu ndi ciwiri ndilo Sabata lakupumula, lopatulika la Yehova; ali yense wogwira nchito tsiku la Sabata aphedwe ndithu.

16 Cifukwa cace ana a Israyeli azisunga Sabata, kucita Sabata mwa mibadwo yao, likhale pangano losatha;

17 ndico cizindikilo cosatha pakati pa Ine ndi ana a Israyeli; pakuti Yehova analenga zam'mwamba ndi dziko lapansi masiku asanu ndi limodzi, napumula tsiku lacisanu ndi ciwiri, naonanso mphamvu.

18 Ndipo atatha iye kulankhula ndi Mose, pa phiri la Sinai, anampatsa magome awiri a mboni, magome amiyala, olembedwa ndi cala ca Mulungu.

32

1 Koma pamene anaona kuti Mose anacedwa kutsika m'phiri, anthuwo anasonkhana kwa Aroni, nanena naye, Ukani, tipangireni milungu yakutitsogolera; pakuti Mose uyu, munthuyu anatikweza kucokera m'dziko la Aigupto, sitidziwa comwe camgwera.

2 Ndipo Aroni ananena nao, Thyolani mphete zagolidi ziri; m'makutu a akazi anu, a ana anu amuna ndi akazi, ndi kubwera nazo kwa ine.

3 Ndipo anthu onse anathyola mphete zagolidi zinali m'makutu mwao, nabwera nazo kwa Aroni.

4 Ndipo anazilandira ku manja ao, nacikonza ndi cozokotera, naciyenga mwana wa ng'ombe; ndipo anati, Siyi milungu yako, Israyeli, imene inakukweza kucokera m'dziko la Aigupto.

5 Pakuciona Aroni, anamanga guwa la nsembe patsogolo pace; ndipo Aroni anapfuula nati, Mawa aliko madyerero a Yehova.

6 Ndipo m'mawa mwace anauka mamawa, nafukiza nsembe zopsereza, nabwera nazo nsembe zamtendere; ndi anthu anakhala pansi kudya ndi kumwa, nauka kusewera.

7 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Muka, tsikatu, pakuti anthu ako udakwera nao kucokera m'dziko la Aigupto wadziipsa;

8 wapatuka msanga njira imene ndinawauza; wadzinyengera mwana wa ng'ombe, namgwadira, namphera nsembe, nati, Siyi milungu yako, Israyeli, imene inakukweza kucokera m'dziko la Aigupto,

9 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Ndawapenya anthu awa, taona, ndiwo anthu opulupudza;

10 ndipo tsopano ndileke, kuti ndipse mtima pa awo ndi kuwatha, ndi kukuza iwe ukhale mtundu waukuru.

11 Ndipo Mose anapemba kwa Yehova Mulungu wace, nati, Yehova, mtima wanu upserenji pa anthu anu, amene munawaturutsa m'dziko la Aigupto ndi mphamvu yaikuru, ndi dzanja lolimba?

12 Akaneneranji Aaigupto; ndi kuti, Anawaturutsa coipa, kuti awaphe m'mapiri, ndi kuwatha pankhope pa dziko lapansi? Pepani, lekani coipaco ca pa anthu anu.

13 Kumbukilani Abrahamu, Isake ndi Israyeli, atumiki anu, amene munawalumbirira ndi kudzichula nokha, amene munanena nao, Ndidzacurukitsa mbeu zanu ngati nyenyezi za kuthambo, ndi dziko ili lonse ndanenali ndidzapatsa mbeu zanu, likhale colowa cao nthawi zonse.

14 Ndipo Yehova analeka coipa adanenaci, kuwacitira anthu ace.

15 Ndipo Mose anatembenuka, natsika m'phirimo, magome awiri a mboni ali m'dzanja lace; magome olembedwa kwina ndi kwina; analembedwa mbali yina ndi inzace yomwe.

16 Ndipo magomewo ndiwo nchito ya Mulungu, kulembaku ndiko kulemba kwa Mulungu, kozokoteka pa magomewo.

17 Ndipo pamene Yoswa anamva phokoso la kupfuula kwa anthu, anati kwa Mose, Kuli phokoso la nkhondo kucigono.

18 Koma iye anati, Phokosoli sindilo la kupfuula kwa olakika, kapena la kupfuula kwa opasuka; koma phokoso ndikumvali ndilo la othirirana mang'ombe.

19 Ndipo kunali, pamene anayandikiza cigono, anaona mwana wa ng'ombeyo ndi kubvinako; ndipo Mose anapsa mtima, nataya magome ali m'manja mwace, nawaswa m'tsinde mwa phiri.

20 Ndipo anatenga mwana wa ng'ombe anampangayo, namtentha ndi moto, nampera asalale, namwaza pamadzi, namwetsako ana a Israyeli.

21 Ndipo Mose anati kwa Aroni, Anthu awa anakucitiranji, kuti iwe watengera iwo kulakwa kwakukuru kotere?

22 Ndipo Aroni anati, Asapse mtima mbuye wanga; udziwa anthuwa kuti akhumba coipa.

23 Pakuti ananena nane, Tipangireni milungu yakutitsogolera; popeza Mose uyu, munthuyu anatikweza kucokera m'dziko la Aigupto, sitidziwa comwe camgwera.

24 Ndipo ndinanena nao, Ali yense ali naye golidi amthyole; ndipo anandipatsa; ndipo ndinaciponya m'moto, ndimo anaturukamo mwana wa ng'ombe uyu.

25 Ndipo pamene Mose anaona kuti anthu anamasuka, popeza Aroni adawamasula kuti awatonze adani ao,

26 Mose anaima pa cipata ca cigono, nati, Onse akubvomereza Yehova, adze kwa ine. Pamenepo ana amuna onse a Levi anasonkhana kwa iye,

27 Ndipo ananena nao, Atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Yense amange lupanga lace m'cuuno mwace, napite, nabwerere kuyambira cipata kufikira cipata, pakati pa cigono, naphe yense mbale wace, ndi yense bwenzi lace, ndi yense mnansi wace.

28 Ndipo ana a Levi anacita monga mwa mau a Mose; ndipo adagwa tsiku lija anthu ngati zikwi zitatu.

29 Popeza Mose adati, Mdzazireni Yehova manja anu lero, pakuti yense akhale mdani wa mwana wace wamwamuna, ndi mdani wa mbale wace; kuti akudalitseni lero lino.

30 Ndipo kunali m'mawa mwace, kuti Mose anati kwa anthu, Mwacimwa kucimwa kwakukulu; koma ndikwera kwa Yehova tsopano, kapena ndidzacita cotetezera ucimo wanu.

31 Ndipo Mose anabwerera kumka kwa Yehova, nati, Ha! pepani, anthu awa anacimwa kucimwa kwakukuru, nadzipangira milungu yagolidi.

32 Koma tsopano, kapena mudzakhululukira kucimwa kwao; koma ngati mukana, mundifafanizetu, kundicotsa m'buku lanu limene munalembera,

33 Ndipo Yehova anati kwa Mose, iye amene wandicimwira, ndifafaniza yemweyo kumcotsa m'buku langa.

34 Ndipo tsopano, muka, tsogolera anthu kumka nao kumene ndinakuuza; taona, mthenga wanga akutsogolera; koma tsiku lakuwazonda Ine ndidzawalanga cifukwa ca kucimwa kwao.

35 Ndipo Yehova anakantha anthu, cifukwa anapanga mwana wa ng'ombe amene Aroni anapanga.

33

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Muka, kwera kucokera kuno, iwe ndi anthu amene unawakweza kucokera m'dziko la Aigupto, kumka ku dzikolo ndinalumbirira nalo Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo, ndi kuti, Ndidzapatsa mbeu zako ilo;

2 ndipo ndidzatuma mthenga akutsogolere; ndipo ndidzapitikitsa Akanani, ndi Aamori, ndi Ahiti, ndi Aperizi, Ahivi, ndi Ayebusi;

3 kudziko koyenda mkaka ndi uci ngati madzi; pakuti sindidzakwera pakati pa inu; popeza inu ndinu anthu opulupudza; ndingathe inu panjira.

4 Ndipo pamene anthu anamva mau awa oipa anacita cisoni; ndipo panalibe mmodzi anabvala zokometsera zace.

5 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Nena ndi ana a Israyeli, Inu ndinu anthu opulupudza; ndikakwera kulowa pakati pa inu kamphindi kamadzi, ndidzakuthani; koma tsopano, bvulani zokometsera zanu, kuti ndidziwe comwe ndikucitireni.

6 Ndipo ana a Israyeli anazicotsera zokometsera zao kuyambira pa phiri la Horebe.

7 Ndipo Mose akatenga cihemaco nacimanga kunja kwa cigono, kutari kwa cigono; nacicha, Cihema cokomanako. Ndipo kunakhala kuti yense wakufuna Yehova anaturuka kumka ku cihema cokomanako kunja kwa cigono.

8 Ndipo kunali, pakuturuka Mose kumka ku cihemaco kuti anthu onse anaimirira, nakhala ciriri, munthu yense pakhomo pa hema wace, nacita cidwi pa Mose, kufikira atalowa m'cihemaco.

9 Ndipo kunali, pakulowa Mose m'cihemaco, mtambo njo udafutsika, nuima pakhomo pa cihemaco; ndipo Yehova analankhula ndi Mose.

10 Ndipo anthu onse anaona mtambo njo ulikuima pakhomo pa cihema; ndi anthu onse anaimirira, nalambira, yense pakhomo pa hema wace.

11 Ndipo Yehova ananena ndi Mose kopenyana maso, monga munthu alankhula ndi bwenzi lace. Ndipo anabwerera kumka kucigono; koma mtumiki wace Yoswa, mwana wa Nuni, ndiye mnyamata msinkhu wace, sanacoka m'cihemamo.

12 Ndipo Mose anati kwa Yehova, Taonani, Inu munena ndi ine, Kwera nao anthu awa; koma simunandidziwitsa amene mudzamtuma amuke nane. Koma munati, Ndikudziwa dzina lako, wapezanso ufulu pamaso panga,

13 Ndipo tsopano, ngati ndapeza ufulu pamaso panu, mundidziwitsetu njira zanu, kuti ndikudziweni, ndi kuti ndipeze ufulu pamaso panu; ndipo penyani kuti mtundu uwu ndi anthu anu.

14 Ndipo anati, Nkhope yanga idzamuka nawe, ndipo ndidzakupumuza.

15 Ndipo ananena ndi Iye, Ikapanda kumuka nane nkhope yanu, musatikweze kucokera kuno.

16 Pakuti cidziwfka ndi ciani tsopano kuti ndapeza ufulu pamaso panu, ine ndi anthu anu? Si pakumuka nafe Inu, kuti ine ndi anthu anu tisiyane ndi anthu onse akukhala pa nkhope ya dziko lapansi?

17 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Ici comwe wanenaci ndidzacita; pakuti wapeza ufulu pamaso panga, ndipo ndikudziwa dzina lako.

18 Ndipo anati, Ndionetsenitu ulemerero wanu.

19 Ndipo iye anati, Ndidzapititsa ukoma wanga wonse pamaso pako, ndipo ndidzachula dzina la Yehova pamaso pako; ndipo ndidzacitira ufulu amene ndidzamcitira ufulu; ndi kucitira cifundo amene ndidzamcitira cifundo.

20 Ananenanso, Sungathe kuona nkhope yanga; pakuti palibe munthu adzandiona Ine ndi kukhala ndi moyo.

21 Ndipo Yehova anati, Taona pali Inepo pali malo, ndipo uime pathanthwe;

22 ndipo kudzakhala, pakupitira olemerero wanga, ndidzakuika mu mpata wa thanthwe, ndi kukuphimba ndi dzanja langa, mpaka nditapitira;

23 ndipo pamene ndicotsa dzanja langa udzaona m'mbuyo mwanga; koma nkhope yanga siidzaoneka.

34

1 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Dzisemere magome awiri amiyala onga oyamba aja; ndipo ndidzalembera pa magomewo mau omwewo anali pa magome oyambawo, amene unawaswa.

2 Nukonzekeretu m'mawa, nukwere m'mawa m'phiri la Sinai, nuimepo pamaso panga pamwamba pa phiri.

3 Palibe munthu akwere ndi iwe, asaonekenso munthu ali yense m'phiri monse; ndi zoweta zazing'ono kapena zoweta zazikuru zisadye kuphiri kuno.

4 Ndipo anasema magome awiri a miyala, onga oyamba aja; ndipo Mose anauka mamawa nakwera m'phiri la Sinai, monga Yehova adamuuza, nagwira m'dzanja mwace magome awiri amiyala.

5 Ndipo Yehova anatsika mumtambo, naimapo pamodzi ndi iye, napfuula dzina la Yehova.

6 Ndipo Yehova anapita pamaso pace, napfuula, Yehova, Yehova, Mulungu wacifundo ndi wacisomo, wolekereza, ndi wa ukoma mtima wocuruka, ndi wacoonadi;

7 wakusungira anthu osawerengeka cifundo, wakukhululukira mphulupulu ndi kulakwa ndi kucimwa; koma wosamasula woparamula; wakulangira ana ndi zidzukulu cifukwa ca mphulupulu ya atate ao, kufikira mbadwo wacitatu ndi wacinai.

8 Ndipo Mose anafulumira, naweramira pansi, nalambira.

9 Ndipo anati, Ngati ndapeza ufulu tsopane pamaso panu, Ambuye, ayendetu Ambuye pakati pa ife; pakuti awa ndi anthu opulupudza; ndipo mutikhululukire mphulupulu ndi ucimo wathu, ndipo mutilandire tikhale colowa canu.

10 Ndipo iye anati, Taona, Ine ndicita pangano; ndidzacita zozizwa pamaso pa anthu ako onse, sizinacitika zotere ku dziko lonse lapansi, kapena ku mtundu uti wonse wa anthu; ndipo anthu onse amene uli pakati pao adzaona nchito ya Yehova, pakuti cinthu ndikucitiraci ncoopsa.

11 Dzisungire cimene Ine ndikuuza lero lino: taona, ndiingitsa pamaso pako Aamori ndi Akanani, ndi Ahiti ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi.

12 Dzicenjere ungacite pangano ndi anthu a ku dziko limene umukako, lingakhale msampha pakati panu;

13 koma mupasule maguwa a nsembe ao, ndi kuphwanya zoimiritsa zao, ndi kulikha zifanizo zao;

14 pakuti musalambira mulungu wina; popeza Yehova dzina lace ndiye Wansanje, ali Mulungu wansanje;

15 ungacite pangano ndi iwo okhala m'dzikomo; ndipo angacite cigololo pakutsata milungu yao, nangaphere nsembe milungu yao, ndipo angakuitane wina, nukadye naye nsembe zace;

16 ndipo ungatengereko ana ako amuna ana ao akazi; nangacite cigololo ana ao akazi potsata milungu yao, ndi kucititsa ana anu amuna cigololo potsata milungu yao.

17 Usadzipangire milungu yoyenga.

18 Uzisunga madyerero a mkate wopanda cotupitsa. Uzidya mkate wopanda cotupitsa masiku asanu ndi awiri, monga ndakuuza pa nthawi yonenedwa, m'mwezi wa Abibu; pakuti mwezi wa Abibu unaturuka m'Aigupto.

19 Onse oyambira kubadwa ndi anga; ndi zoweta zanu zonse zazimuna, zoyamba za ng'ombe ndi za nkhosa.

20 Koma woyamba wa buru uzimuombola ndi mwana wa nkhosa; ukapanda kumuombola, uzimthyola khosi. Ana anu amuna oyamba onse uziwaombola. Ndipo asamaoneka pamaso panga opanda kanthu.

21 Masiku asanu ndi limodzi uzigwira nchito, koma lacisanu ndi ciwiri uzipumula; nyengo yakulima ndi nyengo yamasika uzipumula.

22 Ndipo uzicita madyerero a masabata, ndiwo madyerero a zipatso zoyamba za masika a tirigu, ndi madyerero a kututa pakutha pa caka.

23 Amuna ako onse azioneka pamaso pa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israyeli, katatu caka cimodzi.

24 Pakuti ndidzaingitsa mitundu ya anthu pamaso pako, ndi kukulitsa malire ako; ndipo palibe munthu adzakhumba dziko lako, pakukwera iwe kudzaoneka pamaso pa Yehova Mulungu wako katatu caka cimodzi.

25 Usapereke mwazi wa nsembe yanga yophera pamodzi ndi mkate wacotupitsa; ndi nsembe yophera ya madyerero a Paskha asaisiye kufikira m'mawa.

26 Uzibwera nazo zipatso zoyambayamba za nthaka yako ku nyumba ya Yehova Mulungu wako. Usaphika mwana wa mbuzi mu mkaka wa mace.

27 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Ulembere mau awa; pakuti monga mwa mau awa ndapangana ndi iwe ndi Israyeli.

28 Ndipo anakhala pomwepo ndi Yehova masiku makumi anai, usana ndi usiku; sanadya mkate kapena kumwa madzi. Ndipo analembera pa magomewo mau a panganolo, mau khumiwo.

29 Ndipo kunali pakutsika Mose pa phiri la Sinai, ndi magome awiri a mboni m'dzanja lace la Mose, pakutsika iye m'phirimo, Mose sanadziwa kuti khungu la nkhope yace linanyezimira popeza iye adalankhula naye.

30 Ndipo pamene Aroni ndi ana onse a Israyeli anaona Mose, taonani, khungu la nkhope yace linanyezimira; ndipo anaopa kumyandikiza.

31 Koma Mose anawaitana; ndipo Aroni ndi akazembe onse a khamu la anthu anabwera kwa iye; ndipo Mose analankhula nao.

32 Ndipo atatero, ana onse a Israyeli anayandikiza; ndipo iye anawauza zonse Yehova adalankhula naye m'phiri la Sinai.

33 Ndipo Mose atatha kulankhula nao, anaika cophimba pankhope pace.

34 Koma pakulowa Mose pamaso pa Yehova kunena ndi iye, ariacotsa cophimbaco, kufikira akaturuka; ndipo ataturuka analankhula ndi ana a Israyeli cimene adamuuza.

35 Ndipo ana a Israyeli anaona nkhope ya Mose, kuti khungu la nkhope ya Mose linanyezimira; ndipo Mose anaikanso cophimba pankhope pace, kufikira akalowa kulankhula ndi iye.

35

1 Ndipo Mose anasonkhanitsa khamu lonse la ana a Israyeli, nanena nao, Siwa mau amene Yehova anauza, kuti muwacite.

2 Masiku asanu ndi limodzi azigwira nchito; koma tsiku lacisanu ndi ciwiri muliyese lopatulika, Sabata lakupuma la Yehova: ali yense agwira nchito pamenepo, aphedwe,

3 Musamasonkha mota m'nyumba zanu ziri zonse tsiku la Sabata.

4 Ndipo Mose ananena ndi khamu lonse la ana a Israyeli, ndi kuti, Ici ndi cimene Yehova anauza ndi kuti,

5 Mumtengere Yehova copereka ca mwa zanu; ali yense wa mtima womfunitsa mwini abwere naco, ndico copereka ca Yehova;

6 golidi, ndi siliva, ndi mkuwa; ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi;

7 ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, ndi mtengo wasitimu;

8 ndi mafuta akuunikira, ndi zonunkhira za mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma;

9 ndi miyala yasohamu, ndi miyala yoika ya efodi, ndi ya capacifuwa.

10 Ndipo abwere yense wa mtima waluso mwa inu, napange zonse zimene Yehova anauza;

11 kacisi, hema wace, ndi cophimba cace, zokowera zace, ndi matabwa ace, mitanda yace, mizati, nsanamira, ndi nsici zace, ndi makamwa ao;

12 likasa, ndi mphiko zace, cotetezerapo, ndi nsaru yocinga yotseka;

13 gome, ndi mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, ndi mkate woonekera;

14 ndi coikapo nyali ca kuunika, ndi zipangizo zace, ndi nyali zace, ndi mafuta a kuunika;

15 ndi guwa la nsembe lofukizapo, ndi mphiko zace, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsaru yotsekera pakhomo, pa khomo la kacisi;

16 guwa la nsembe yopereza, ndi made amkuwa, mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, mkhate ndi tsinde lace;

17 nsaru zocingira za kubwalo, nsici zace, ndi makamwa ace, ndi nsaru yotsekera ku cipata ca pabwalo;

18 ziciri za cihema, ndi ziciri za kubwalo, ndi zingwe zao;

19 zobvala za kutumikira nazo m'maopatulika, zobvala zopatulika za. Aroni wansembe, ndi zobvala za ana ace, zakugwira nazo nchito ya nsembe.

20 Ndipo khamu lonse la ana a Israyeli linacoka pamaso pa Mose.

21 Ndipo anadza, ali yense wofulumidwa mtima, ndi yense mzimu wace wamfunitsa, nabwera naco copereka ca Yehova, ca ku nchito ya cihema cokomanako, ndi ku utumiki wace wonse, ndi ku zobvala zopatulika.

22 Ndipo anadza amuna ndi akazi, onse akufuna mtima eni ace, nabwera nazo mphete za mphuno, mphete za m'makutu, ndi mphete zosindikizira, ndi zidzingwiri, zonsezi zokometsera zagolidi; inde yense wakupereka kwa Yehova copereka cagolidi.

23 Ndipo ali yense kwao kunapezeka lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ubweya wa mbuzi, ndi zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi zikopa za akatumbu, anabwera nazo.

24 Yense wakupereka copereka ca siliva ndi mkuwa, anabwera naco copereka ca Yehova; ndi yense amene kwao kunapezeka mtengo wasitimu wa ku macitidwe onse a nchitoyi, anabwera nao.

25 Ndi akazi onse a mtima waluso anapota ndi manja ao, nabwera nalo thonje lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

26 Ndi akazi onse ofulumidwa mtima ndi luso anapota ubweyawo wa mbuzi.

27 Ndi akuru anabwera nayo miyala yasohamu, ndi miyala yoti aiike kuefodi, ndi kucapacifuwa;

28 ndi zonunkhira, ndi mafuta akuunikira, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza za pfungo lokoma.

29 Amuna ndi akazi onse a ana a Israyeli amene mitima yao inawafunitsa eni kubwera nazo za ku nchito yonse imene Yehova anauza Ipangike ndi dzanja la Mose, anabwera naco copereka cofuna mwini, kucipereka kwa Yehova.

30 Ndipo Mose anati kwa ana a Israyeli, Taonani, Yehova anaitana, ndi kumchula dzina lace, Bezaleli, mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa pfuko la Yuda;

31 ndipo anamdzaza ndi mzimu wa Mulungu, ndi luso, ndi nzeru, ndi cidziwitso, za m'nchito ziri zonse;

32 kulingirira nchito zaluso, kucita ndi golidi, ndi siliva, ndi mkuwa;

33 ndi kuzokota miyala voikika, ndi kuzokota mitengo, kucita m'nchito ziri zonse zaluso.

34 Ndipo anaika m'mtima mwace kuti alangize ena, iye ndi Aholiabu mwana wa Ahisama, wa pfuko la Dani.

35 Amenewo anawadzaza ndi luso lamtima, lakucita nchito ziri zonse, ya kuzokota miyala, ndi ya mmisiri waluso, ndi ya wopikula ndi lamadzi ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ya muomba, ya iwo akucita nchito iri yonse, ndi ya iwo olingirira nchito yaluso.

36

1 Aholiabu, ndi anthu aluso, amene Yehova adaika luso ndi nzeru m'mtima mwao adziwe macitidwe ace a nchito yonse ya utumiki wace wa malo opatulika, monga mwa zonse adauza Yehova.

2 Ndipo Mose adaitana Bezaleli ndi Aholiabu, ndi anthu onse aluso, amene Yehova adaika luso m'mtima mwao, onse ofulumidwa mtima ayandikize kunchito kuicita.

3 Ndipo analandira kwa Mose copereka conse, cimene ana a Israyeli adabwera naco cikhale ca macitidwe a nchito ya malo opatulika, aipange naco. Koma anaonjeza kubwera nazo kwa iye zopereka zofuna mwini, m'mawa ndi m'mawa.

4 Ndipo aluso onse, akucita nchito yonse ya malo opatulika, anadza onse ndi kusiya nchito yao: analinkucita;

5 nanena ndi Mose, ndi kuti, Anthu alinkubwera nazo zocuruka, zakuposera zoyenera nchito imene Yehova anauza icitike.

6 Ndipo Mose analamulira, ndipo anamveketsa mau mwa cigono conse, ndi kuti, Asaonjezere nchito ya ku copereka ca malo opatulika, ngakhale mwamuna ngakhale mkazi. Tero anawaletsa anthu asabwere nazo zina.

7 Popeza zipangizo zinakwanira nchito yonse icitike, zinatsalakonso.

8 Ndipo onse a mtima waluso mwa iwo akucita nchitoyi anapanga kacisi ndi nsaru zophimba khumi; anaziomba ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi lamadzi; ndi lofiira, ndi lofiira, ndi akerubi, nchito ya mmisiri.

9 Utali wace wa nsaru yophimba imodzi ndiwo mikono makumi awiri kudza isanu ndi itatu, ndi kupingasa kwace kwa nsaru imodzi mikono inai; nsaru zonse zinafanana muyeso wao.

10 Ndipo analumikiza nsaru zisanu yina ndi inzace; nalumikiza nsaru zisanu zina yina ndi inzace.

11 Ndipo anaika magango ansaru yamadzi m'mphepete mwace mwa nsaru imodzi ku mkawo wa cilumikizano; nacita momwemo m'mphepete mwace mwa nsaru ya kuthungo, ya cilumikizano caciwiri.

12 Anaika magango makumi asanu pa nsaru imodzi, naikanso magango makumi asanu m'mphepete mwace mwa nsaru ya cilumikizano cina; magango anakomanizana lina ndi linzace.

13 Ndipo anazipanga zokowera makumi asanu zagolidi, namanga nsaru pamodzi ndi zokowerazo; ndipo kacisi anakhala mmodzi.

14 Ndipo anaomba nsaru zophimba za ubweya wa mbuzi zikhale hema pamwamba pa kacisi; anaomba nsaru zophimba khumi ndi imodzi.

15 Utali wace wa nsaru imodzi ndiwo mikono makumi atatu, ndi kupingasa kwace kwa nsaru imodzi ndiko mikono inai; nsaru khumi ndi imodzi zinafanana muyeso wao.

16 Ndipo anamanga pamodzi nsaru zisanu pa zokha, ndi nsaru zisanu ndi imodzi pa zokha.

17 Ndipo anapanga magango makumi asanu m'mphepete mwa nsaru imodzi, ya kuthungo, ya cilumikizano, naika magango makumi asanu m'mphepete mwa nsaru ya kuthungo, ya cilumikizano cina.

18 Ndipo anapanga zokowera makumi asanu zamkuwa kumanga pamodzi hemalo, kuti likhale limodzi.

19 Ndipo anasokera hemalo cophimba ca zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi cophimba ca zikopa za akatumbu pamwamba pace.

20 Ndipo anapanga matabwa a kacisi, oimirika, a mtengo wasitimu.

21 Utali wace wa thabwa limodzi ndiwo mikono khumi, ndi kupingasa kwace kwa thabwa limodzi ndiko mkono ndi hafu.

22 Pa thabwa limodzi panakhala mitsukwa iwiri, yomangika pamodzi; anawapanga momwemo matabwa onse a kacisi.

23 Ndipo anapanga matabwa a kacisi; matabwa makumi awiri a ku mbali ya kumwela, kumwela;

24 napanga makamwa makumi anai pansi pamatabwa makumi awiri; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi kwa mitsukwa yace iwiri, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina kwa mitsukwa yace iwiri.

25 Ndi ku mbali yina ya kacisi, mbali ya kumpoto, anapanga matabwa makumi awiri, ndi makamwa ao makumi anai asiliva;

26 makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina.

27 Ndi ku mbali ya kumbuyo ya kacisi kumadzulo anapanga matabwa asanu ndi limodzi.

28 Anapanganso matabwa awiri a ku ngondya za kacisi, m'mbali zace ziwirio

29 Ndipo anaphatikizika pamodzi patsinde, naphatikizilca pamodzi pamutu pace ndi mphete imodzi; anatero nao onse awiri pa ngondya ziwiri.

30 Ndipo panali matabwa asanu ndi atatu ndi makamwa ao asiliva, makamwa khumi kudza asanu ndi limodzi; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi.

31 Ndipo anapanga mitanda ya mtengo wasmmu; Isanu ya matabwa a pa mbali yina ya kacisi,

32 ndi mitanda isanu ya matabwa a pa mbali inzace ya kacisi, ndi mitanda lsanu ya matabwa a kacisi ali pa mbali ya kumadzulo.

33 Ndipo anapititsa mtanda wa pakatipo, pakati pa matabwa kufikira kuthungo.

34 Ndipo anakuta matabwa ndi golidi, napanga mphete zao zagolidi zikhale zopisamo mitandayo, nakuta mitandayo ndi golidi.

35 Ndipo anaomba nsaru yocinga ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa; anaciomba ndi akerubi nchito ya mmisiri.

36 Ndipo anaipangira mizati inai yasitimu, nazikuta ndi golidi; zokowera zao zinali zagolidi; ndipo anaziyengera makamwa anai asiliva.

37 Ndipo anaomba nsaru yotsekera pa khomo la cihemaco, ya lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, nchito ya wopikula;

38 ndi nsamamira zace zisanu ndi zokowera zao; nakuta mitu yao ndi mitanda yao ndi golidi; ndi makamwa ao asanu anali amkuwa.

37

1 Ndipo Bezaleli anapanga likasa la mtengo wasitimu; utali wace mikono iwiri ndi hafu, ndi kupingasa kwace mkono ndi hafu, ndi msinkhu wace mkono ndi hafu;

2 ndipo analikuta ndi golidi woona m'kati ndi kunja, nalipangira mkombero wagolidi pozungulira pace.

3 Ndipo analiyengera mphete zinai zagolidi pa miyendo yace inai; mphete ziwiri pa mbali yace imodzi, ndi mphete: ziwiri pa mbali yace yina.

4 Ndipo anapanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndi golidi.

5 Ndipo anapisa mphiko m'mphetezo pa mbali zace za likasalo, kuti anyamulire nazo likasa.

6 Ndipo anapanga cotetezerapo ca golidi woona; utali wace mikono iwiri ndi hafu, ndi kupingasa kwace mkono ndi hafu.

7 Anapanganso akerubi awiri agolidi; anacita kuwasula mapangidwe ace, pa mathungo ace swiri a coteteze rapo;

8 kerubi mmodzi pa mbali yace imodzi, ndi kerubi wilia pa mbali yace yina; anapanga akerubi ocokera m'cotetezerapo, pa mathungo ace awiri.

9 Ndipo akerubi anafunyulira mapiko ao m'mwamba, ndi kuphimba cotetezerapo ndi mao piko ao, ndi nkhope zao zopeoyana; zinapenya kucotetezerapo nkhope zao.

10 Ndipo anapanga gome la mtengo wasitimu; utali wace mikono iwiri, ndi kupingasa kwace mkono limodzi, ndi msinkhu wace mkono ndi hafu;

11 ndipo analikuta ndi golidi woona, nalipangira mkombero wagolidi pozungulira pace.

12 Analipangiranso mitanda pozungulirapo, yoyesa cikhato m'kupingasa kwace, ndi pamitanda pace pozungulira anapangirapo mkombero wagolidi.

13 Ndipo analiyengera mphete zinai zagolidi, naika mphetezo pa ngondya zace zinai zokhala pa miyendo yace inai.

14 Mphetezo zinali pafupi pa mitanda, zikhale zopisamo mphiko kunyamulira nazo gomelo.

15 Ndipo anapanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndigolidi, kunyamulira nazo gomelo.

16 Anapanganso zipangizo za gomelo, mbale zace, ndi zipande zace, ndi mitsuko yace, ndi zikho zace zakuthira nazo, za golidi woona.

17 Ndipo anapanga coikapo nyali ca golidi woona; mapangidwe ace a coikapo nyalico anacita cosula, tsinde lace ndi thupi lace, zikho zace, mitu yace, ndi maluwa ace zinakhala zocokera m'mwemo;

18 ndi m'mbali zace munaturuka mphanda zisanu ndi imodzi; mphanda zitatu za coikapo nyali zoturuka m'mbali yace imodzi, ndi mphanda zitatu za coikapo nyali zoturuka m'mbali yace yina;

19 pa mphanda imodzi panali zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi luwa; ndi pa mphanda yina zikho zitatu zopangika ngati katungurume, mutu ndi luwa; zinatero mphanda zisanu ndi imodzi zoturuka m'coikapo nyali.

20 Ndipo pa coikapo nyali comwe panali zikho zinai zopangika ngati katungurume, mitu yace ndi maluwa ace;

21 ndipo panali mutu pansi pa mphanda ziwiri, zoturuka m'mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri, zoturuka m'mweno, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri, zoturuka m'mwemo, inatero pa mphanda zisanu ndi imodzi zocokera m'mwemo.

22 Mitu yao ndi mphanda zao zinaturuka m'mwemo; conseci cinali cosulika pamodzi ca golidi woona.

23 Ndipo anapanga nyali zace zisanu ndi ziwiri ndi mbano zace, ndi zoolera zace, za golidi woona.

24 Anacipanga ici ndi zipangizo zace zonse za talente wa golidi woona.

25 Ndipo anapanga guwa la nsembe lofukizapo la mtengo wasitimu; utali wace mkono, ndi kupingasa kwace mkono, lampwamphwa; ndimsinkhu wace mikono iwiri; nyanga zace zinaturuka m'mwemo.

26 Ndipo analikuta ndi golidi woona, pamwamba pace, ndi mbali zace pozungulira, ndi nyanga zace; ndipo analipangira mkombero wagolidi pozungulira pace.

27 Ndipo analipangira mphete ziwiri zagolidi pansi pa mkombero wace, pa ngondya zace ziwiri, pa mbali zace ziwiri, zikhale zopisamo mphiko kulinyamulira nazo.

28 Ndipo anazipanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndi golidi.

29 Anapanganso mafuta opatulika akudzoza nao, ndi cofukiza coona ca pfungo lokoma, mwa macitidwe a wosanganiza.

38

1 Ndipo anapanga guwa la nsembe yopsereza la mtengo wasitimu; utali wace mikono isanu, ndi kupingasa kwace mikono isanu, lampwamphwa; ndi msinkhu wace mikono itaru.

2 Ndipo anapanga nyanga zace pa ngondya zace zinai; nyanga zace zinakhala zoturuka m'mwemo; ndipo analikuta ndi mkuwa.

3 Anapanganso zipangizo zonse za guwalo, zotayira, ndi zoolera, ndi mbale zowazira, ndi mitungo, ndi zoparira moto; zipangizo zace zonse anazipanga zamkuwa.

4 Ndipo anapangira guwa La nsembelo made, malukidwe ace nja mkuwa, pansi pa matso ace wakulekeza pakati pace.

5 Ndipo anayengera mathungo anai a made amkuwawo mphete zinai, zikhale zopisamo mphiko.

6 Napanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndi mkuwa.

7 Ndipo anapisa mphikozo m'zimphetemo pa mbali za guwa la nsembe, kulinyamulira nazo; analipanga ndi matabwa, lagweregwere.

8 Ndipo anapanga mkhate wamkuwa, ndi tsinde lace lamkuwa, wa akalirole a akazi otumikira, akutumikira pa khomo la cihema cokomanako.

9 Ndipo anapanga bwalo; pa mbali ya kumwela, kumwela, nsaru zocingira za pabwalo zinali za bafuta wa thonje losansitsa, mikono zana limodzi;

10 nsici zace makumi awiri, ndi makamwa ao makumi awiri, amkuwa; zokowera za nsici ndi mitanda yace zasiliva.

11 Ndi pa mbali ya kumpoto mikono zana limodzi, nsici zace makumi awiri, nw makamwa ace makumi awiri, amkuwa; zokowera za nsici ndi mitanda yace yasiliva.

12 Ndi pa mbali ya kumadzulo panali nsaru zocingira za mikono makumi asanu, nsid zace khumi, ndi makamwa ace khumi; zokowera za nsici ndi mitanda yace yasiliva.

13 Ndi pa mbali ya kum'mawa, kum'mawa, mikono makumi asanu.

14 Nsaru zocingira za pa mbali imodzi ya cipata nza mikono khumi ndi isanu; nsici zace zitatu, ndi makamwa ace atatu;

15 momwemonso pa mbali yina: pa mbali yino ndi pa mbali yina ya cipata ca pabwalo panali nsaru zocingira za mikono khumi ndi isanu; nsici zace zitatu, ndi makamwa ace atatu.

16 Nsaru zocingira zonse za pabwalo pozungulira zinali za bafuta wa thonje losansitsa.

17 Ndipo makamwa a nsici anali amkuwa; zokowera za nsici ndi mitanda Iyace zasiliva; ndi zokutira mitu yace zasiliva; ndi nsici zonse za pabwalo zinagwirana pamodzi ndi siliva.

18 Ndi nsaru yotsekera pa cipata ca pabwalo ndiyo nchito ya wopikula, ya lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa; utali wace mikono makumi awiri, ndi msinkhu wace mu kupingasa kwace mikono isanu, yolingana ndi nsaru zocingira za pabwalo.

19 Ndi nsici zace zinali zinai, ndi makamwa ace anai, amkuwa; zokowera zace zasiliva, ndi zokutira mitu yace ndi mitanda yace zasiliva.

20 Ndi ziciri zonse za cihema, ndi za bwalo lace pozungulira, nza mkuwa.

21 Ici ndi ciwerengo ca zinthu za cihema, cihema ca mboni, monga anaziwerenga, monga mwa mau a Mose, acite nazo Alevi; anaziwerenga Itamara, mwana wa Aroni wansembe.

22 Ndipo Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huri, wa pfuko la Yuda, anapanga zonse zimene Mulungu adauza Mose.

23 Ndi pamodzi naye Aholiabu, mwana wa Ahisama, wa pfuko la Dani, ndiye wozokota miyala, ndi mmisiri waluso, ndiponso wopikula ndi lamadzi ndi lofiira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

24 Golidi yense anacita naye mu nchito yonse ya malo opatulika, golidi wa coperekaco, ndico matalente makumi awiri kudza asanu ndi anai, ndi masekeli mazana asanu ndi awiri, kudza makumi atatu, monga mwa sekeli wa malo opatulika.

25 Ndipo siliva wa iwo owerengedwa a khamulo ndiwo matalente zana limodzi, ndi masekeli cikwi cimodzi, kudza mazana asanu ndi awiri, mphambu makumi asanu ndi awiri kudza asanu, kuyesa sekeli wa malo opatulika;

26 munthu mmodzi anapereka beka, ndiwo limodzi la magawo awiri la sekeli, kuyesa sekeli wa malo opatulika, anatero onse akupita kumka kwa owerengedwawo, kuyambira munthu wa zaka makumi awiri ndi oposa, ndiwo anthu zikwi mazana asanu ndi limodzi kudza zitatu, ndi mazana asanu mphambu makumi asanu.

27 Ndipo matalente zana limodzi a siliva ndiwo a kuyengera makamwa a malo opatulika, ndi makamwa a nsaru yocinga; makamwa zana limodzi matalente zana limodzi, talente limodzi kamwa limodzi.

28 Ndipo anapanga zokowera za mizati nsanamira ndi nsici ndi masekeli aja cikwi cimodzi kudza mazana asanu ndi awiri mphambu asanu, nakuta mitu yace, nazigwirizitsana pamodzi.

29 Ndi mkuwa wa coperekaco ndiwo matalente makumi asanu ndi awiri, ndi masekeli zikwi ziwiri kudza mazana anai.

30 Ndipo anapanga nao makamwa a pa khomo la cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe lamkuwa, ndi made ace amkuwa, ndi zipangizo zonse za guwa la nsembe,

31 ndi makamwa a pabwalo pozungulira, ndi makamwa a ku cipata ca pabwalo, ndi ziciri zonse za cihema, ndi ziciri zonse za pabwalo pozungulira.

39

1 Ndipo anaomba zobvala zakutumikira nazo ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, atumikire nazo m'malo opatulika, naomba zobvala zopatulika za Aroni; monga Yehova adamuuza Mose.

2 Ndipo anaomba efodi wa golidi, lamadzi, lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

3 Ndipo anasula golidi waphanthiphanthi, nalemba nsambo, kuti amuombe pamodzi ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, nchito ya mmisiri.

4 Anapangira efodi zapamapewa zolumikizana; pa nsonga ziwirizo anamlumikiza.

5 Ndi mpango wa efodi wokhala pamenepo, wakummanga nao unali woombera kumodzi wa ciombedwe comweci; wa golidi, ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa; monga Yehova adauza Mose.

6 Ndipo anakonza miyala yasohamu, yogwirika m'zoikamo zagolidi, yoloca ngati malocedwe a cosindikizira, ndi maina a ana a lsrayeli.

7 Ndipo anaiika pa zapamapewa za efodi, ikhale miyala ya cikumbutso kwa ana a Israyeli; monga Yehova adamuuza Mose.

8 Ndipo anaomba capacifuwa, nchito ya mmisiri, monga maombedwe ace a efodi; ca golidi, lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

9 Cinakhala camowamphwa; anaciomba capacifuwa copindika; utali wace cikhato cimodzi, ndi kupingasa kwace cikhato cimodzi, cinakhala copindika.

10 Ndipo anaika pomwepo mizere inai ya miyala; mzere wa odemu, pitida, ndi bareketi, ndiyo ya mzere woyamba.

11 Ndi mzere waciwiri wa nofeki, safiri, ndi yahalomu.

12 Ndi mzere wacitatu wa lesemu, sibu, ndi akalama.

13 Ndi mzere wacinai wa tarisisi, sohamu, ndi yasefe; inakhala yogwirika ndi golidi maikidwe ace.

14 Ndipo miyalayi inakhala monga mwa maina a ana a Israyeli, khumi ndi awiri, monga mwa maina ao; ngati malocedwe a cosindikizira, yonse monga mwa maina ace, kwa mafuko khumi ndi awiriwo.

15 Ndipo anapangira pacapacifuwa maunyolo ngati zingwe, nchito yopota ya golidi woona.

16 Anapanganso zoikamo ziwiri zagolidi, ndi mphete ziwiri zagolidi; naika mphete ziwirizo pa nsonga ziwiri za capacifuwa.

17 Ndipo anamanga maunyolo awiri opota agolidi pa mphete ziwiri pa nsonga za capacifuwa.

18 Ndi nsonga zace ziwiri zina za maunyolo awiri opotawo anazimanga pa zoikamo ziwiri, nazimanga pa zapamapewa za efodi, m'tsogolo mwace.

19 Ndipo anapanga mphete ziwiri zagolidi, naziika pa nsonga ziwiri za capacifuwa, m'mphepete mwace m'katimo, pa mbali ya kuefodi.

20 Ndipo anapanga mphete ziwiri zagolidi, naziika pa zapamapewa ziwiri za efodi pansi pace, pa mbali yace ya kutsogolo, pafupi pa msoko wace, pamwamba pa mpango wa efodi.

21 Ndipo anamanga capacifuwa pa mphete zace ndi mphete za efodi ndi mkuzi wamadzi, kuti cikhale pa mpango wa efodi, ndi kuti capacifuwa cisamasuke paefodi; monga Yehova anamuuza Mose.

22 Ndipo anaomba mwinjiro wa efodi, nchito yoomba ya lamadzi lokha;

23 ndi pakati pace polowa mutu, ngati polowa pa maraya ocingirizira, ndipo anabinyira pozungulira polowa pace, pangang'ambike.

24 Napangira pa mkawo wa mwinjiro makangaza a lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.

25 Ndipo anapanga miriu ya golidi woona, napakiza miriu ndi makangaza, pa mkawo wa mwinjiro pozungulira, popakiza ndi makangaza.

26 Mliu ndi khangaza, mliu ndi khangaza pa mkawo wa mwinjiro pozungulira, kutumikira nazo; monga Yehova anamuuza Mose.

27 Ndipo anaomba maraya a bafuta, a nchito yoomba, a Aroni, ndi a ana ace amuna,

28 ndi nduwira va bafuta wa thonje losansitsa, ndi akapal okometsetsa a bafuta wa thonje losansitsa, ndi zobvala za kumiyendo za bafuta wa thonje losansitsa,

29 ndi mpango wabafuta wa thonje losansitsa, ndi lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, nchito ya wopikula; monga Yehova adamuuza Mose.

30 Ndipo anapanga phanthiphanthi wa korona wopatulika wa golidi woona, nalembapo lemba, ngati malocedwe a cosindikizira, KUPATULIKIRA YEHOVA.

31 Namangako mkuzi wamadzi, kuumanga nao pamwamba pa nduwira; monga Yehova adamuuza Mose.

32 Potero anatsiriza nchito yonseya kacisi wa cihema cokomanako; ndipo ana a Israyeli adacita monga mwa zonse Yehova adamuuza Mose, anacita momwemo.

33 Ndipo anabwera naye kacisi kwa Mose, cihemaco, ndi zipangizo zace zonse, zokowera zace, matabwa ace, mitanda yace, ndi mizati yace, nsanamira zace ndi nsici zace, ndi makamwa ace;

34 ndi cophimba ca zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiirira, ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi nsaru yocinga yotsekera;

35 likasa la mboni, ndi mphiko zace, ndi cotetezerapo;

36 gomelo, zipangizo zace zonse, ndi mkate woonekera;

37 coikapo nyali coona, nyali zace, ndizo nyali zimakonzekazi, ndi zipangizo zace zonse, ndi mafuta a kuunikira;

38 ndi guwa la nsembe lagolidi, ndi mafuta odzoza, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsaru yotsekera pa khomo la cihemaco;

39 guwa la nsembe lamkuwa, ndi made ace amkuwa, mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, mkhate ndi tsinde lace;

40 nsaru zocingira za pabwalo, osici zace, ndi makamwa ace, ndi nsaru yotsekera pa cipata ca pabwalo, zingwe zace, ndi ziciri zace, ndi zipangizo zonse za nchito ya kacisi, za ku cihema cokomanako;

41 zobvala zokoma za kutumikira nazo m'malo opatulika, ndi zobvala zopatulika za Aroni wansembe, ndi zobvala za ana ace, kucita nazo nchito ya usembe.

42 Monga mwa zonse Yehova adamuuza Mose, momwemo ana a Israyeli anacita nchito zonse.

43 Ndipo Mose anaona nchito zonse, ndipo, taonani, adaicita monga Yehova adamuuza, momwemo adacita. Ndipo Mose anawadalitsa.

40

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2 Tsiku loyamba la mwezi woyamba ukautse kacisi wa cihema cokomanako.

3 Ndipo ukaikemo likasa la mboni, nucinge likasalo ndi nsaru yocingayo.

4 Ulongenso gomelo, nukonzerepo zokonzera zace; ulongenso coikapo nyalico, ndi kuyatsa nyali zace.

5 Ndipo ukaike guwa la nsembe lofukizapo lazolidi cakuno ca likasa la mboni, numange pakacisi nsaru yotsekera pakhomo.

6 Ndipo ukaike guwa la nsembe yopsereza kunja kwa khomo la kacisi wa cihema cokomanako.

7 Ukaikenso mkhate pakati pa cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe, ndi kuthiramo madzi.

8 Ndipo ukamange mpandawo pozungulira, ndi kupacika nsaru yotsekera pa cipata ca pabwalo.

9 Pamenepo ukatenge mafuta odzoza, ndi kudzoza nao kacisi, ndi zonse ziri m'mwemo, ndi kumpatula, ndi zipangizo zace zonse; ndipo adzakhala wopatulika.

10 Ndipo udzoze guwa la nsembe yopsereza, ndi zipangizo zace zonse, ndi kulipatula guwalo; ndipo guwalo lidzakhala lopatulikitsa.

11 Udzozenso mkhate ndi tsinde lace, ndi kuupatula.

12 Ndipo ubwere nao Aroni ndi ana ace amuna ku khomo la cihema cokomanako, ndi kuwasambitsa ndi madzi.

13 Nubveke Aroni cobvala zopatulikazo; ndi kumdzoza, ndi kumpatwa andicitire Ine nchito ya nsembe.

14 Ndipo ubwere nao ana ace amuna ndi kuwabveka maraya am'kati;

15 nuwadzoze, monga unadzoza atate wao, kuti andicitire nchito ya nsembe; ndi kudzozedwa kwao kuwakhalire unsembe wosatha mwa mibadwo yao.

16 Anatero Mose; monga mwa zonse Yehova adamuuza, momwemo anacita.

17 Ndipo kunali, mwezi woyamba wa caka caciwiri, tsiku loyamba la mwezi, anautsa kacisi.

18 Ndipo Mose anautsa kacisi, nakhazika makamwa ace, naimika matabwa ace, namangapo mitanda yace, nautsa mizati ndi nsanamira zace.

19 Ndipo anayalika hema pamwamba pa kacisi, naika cophimba ca cihema pamwamba pace; monga Yehova adamuuza Mose.

20 Ndipo anatenga mboniyo, naiika mlikasa, napisa mphiko palikasa, naika cotetezerapo pamwamba pa likasa;

21 nalowa nalo likasa m'kacisi, napacika nsaru yocinga, nacinga likasa la mboni; monga Yehova adamuuza Mose.

22 Ndipo anaika gomelo m'cihema cokomanako, pa mbali ya kumpoto ya kacisi, kunja kwa nsaru yocinga.

23 Nakonzerapo mkate pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

24 Ndipo anaika coikapo nyali m'cihema cokomanako, popenyana ndi gome, pa mbali ya kumwela ya kacisi.

25 Nayatsa nyalizo pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

26 Ndipo anaika guwa la nsembe lagolidi m'cihema cokomanako cakuno ca nsaru yocinga;

27 nafukizapo cofukiza ca pfungo lokoma; monga Yehova adamuuza Mose.

28 Ndipo anapacika kukacisi nsaru yotsekera pakhomo.

29 Ndipo anaika guwa la nsembe yopsereza pa khomo la kacisi wa cihema cokomanako, natenthapo nsembe yopsereza, ndi nsembe yaufa; monga Yehova adamuuza Mose.

30 Ndipo anaika mkhate pakati pa cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe; nathiramo madzi osamba.

31 Ndipo Mose ndi Aroni ndi ana ace amuna anasamba manja ao ndi mapazi ao m'menemo;

32 pakulowa iwo m'cihema cokomanako, ndi pakuyandikiza guwa la nsembe anasamba; monga Yehova adamuuza Mose.

33 Ndipo anautsa mpanda pozungulira pa cihema ndi guwa la nsembe, napacika nsaru yotsekera pa cipata ca pabwalo. Momwemo Mose anatsiriza nchitoyi.

34 Pamenepo mtambo unaphimba cihema cokomanako, ndi ulemerero wa Yehova unadzaza kacisiyo.

35 Ndipo Mose sanathe kulowa m'cihema cokomanako, popeza mtambo unakhalabe pamenepo; ndi ulemerero wa Yehova unadzaza kacisi.

36 Ndipo pakukwera mtambo kucokera kukacisi, ana a Israyeli amayenda maulendo ao onse;

37 koma ukapanda kukwera mtambo, samayenda ulendo wao kufikira tsiku loti wakwera.

38 Pakuti mtambo wa Yehova unakhala pakacisi msana, ndi usiku munali moto m'menemo, pamaso pa mbumba yonse ya Israyeli, m'maulendo ao onse.