1 PACIYAMBI Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
2 Dziko lapansi ndipo linali lopanda kanthu; ndipo mdima unali pamwamba pa nyanja; ndipo mzimu wa Mulungu unaliokufungatira pamwamba pa madzi.
3 Ndipo anati Mulungu, Kuyere; ndipo kunayera.
4 Ndipo anaona Mulungu kuti kuyerako kunali kwabino: ndipo Mulungu analekanitsa kuyera ndi mdima.
5 Ndipo Mulungu anacha kuyerako Usana, ndi mdimawo anaucha Usiku. Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku loyamba.
6 Ndipo anati Mulungu, Pakhale thambo pakati pa madzi, lilekanitse madzi ndi madzi.
7 Ndipo Mulungu anapanga thambo, nalekanitsa madzi anali pansi pa thambolo ndi madzi analf pamwamba pa thambolo: ndipo kunatero.
8 Ndipo Mulungu analicha thambolo Kumwamba. Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku laciwiri.
9 Ndipo anati Mulungu, Madzi a pansi pa kumwamba asonkhane pamodzi pa malo amodzi, uoneke mtunda: ndipo kunatero.
10 Ndipo Mulungu adaucha mtundawo Dziko lapansi; kusonkhana kwa madziko ndipo adaucha Nyanja: ndipo anaona Mulungu kuti kunali kwabwino.
11 Mulungu ndipo anati, Dziko lapansi limere maudzu, therere lobala mbeu, ndi mtengo wazipatso wakubala zipatso monga mwa mtundu wace, momwemo muli mbeu yace, pa dziko lapansi: ndipo kunatero.
12 Ndipo dziko lapansi linamera maudzu, therere lobala mbeu monga mwa mtundu wace, ndi mtengo wakubala zipatso, momwemo muli mbeu yace, monga mwa mtundu wace; ndipo anaona Mulungu kuti kunali kwabwino.
13 Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku lacitatu.
14 Ndipo Mulungu anati, Pakhale zounikira pa thambo la kumwamba, zakulekanitsa usana ndi usiku; zikhale zizindikiro ndi nyengo, ndi masiku, ndi zaka;
15 zikhale zounikira m'thambo la kumwamba, kuti ziunikire pa dziko lapansi; ndipo kunatero.
16 Ndipo Mulungu anapanga zounikira zazikuru ziwiri; counikira cacikuru cakulamulira usana, counikira cacing'ono cakulamulira usiku, ndi nyenyezi zomwe.
17 Mulungu ndipo adaika zimenezo m'thambo la kumwamba, kuti ziunikire pa dziko lapansi,
18 nizilamulire usana ndi usiku, nizilekanitse kuyera ndi mdima: ndipo anaona Mulungu kuti kunali kwabino.
19 Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku lacinai.
20 Ndipo anati Mulungu, Madzi abale zocuruka zamoyo zoyendayenda, ndi mbalame ziuluke pamwamba pa dziko lapansi ndi pamlengalenga.
21 Mulungu ndipo adalenga zinsomba zazikuru ndi zoyendayenda zamoyo zakucuruka m'madzi mwa mitundu yao, ndi mbalame zamapiko, yonse monga mwa mtundu wace: ndipo anaona Mulungu kuti kunali kwabwino.
22 Mulungu ndipo anadalitsa zimenezo, nati, Zibalane, zicuruke, zidzaze madzi a m'nyanja, ndi mbalame zicuruke pa dziko lapansi.
23 Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku lacisanu.
24 Ndipo adati Mulungu, Dziko lapansi libale zamoyo monga mwa mitundu yao, ng'ombe, ndi zokwawa, ndi zinyama za dziko lapansi monga mwa mitundu yao: ndipo kunatero.
25 Ndipo Mulungu anapanga zinyama za dziko lapansi monga mwa mitundu yao; ndi ng'ombe monga mwa mtundu wace, ndi zonse zakukwawa pansi monga mwa mitundu yao; ndipo Mulungu anaona kuti kunali kwabwino.
26 Ndipo anati Mulungu, Tipange munthu m'cifanizo cathu, monga mwa cikhalidwe cathu: alamulire pa nsomba za m'nyanja, ndi pa mbalame za m'mlengalenga, ndi pa ng'ombe, ndi pa dziko lonse lapansi, ndi pa zokwawa zonse zakukwawa pa dziko lapansi.
27 Mulungu ndipo adalenga munthu m'cifanizo cace, m'cifanizo ca Mulungu adamlenga iye; adalenga iwo mwamuna ndi mkazi.
28 Mulungu ndipo anadalitsa iwo, ndipo adati kwa iwo, Mubalane, mucuruke, mudzaze dziko lapansi, muligonjetse: mulamulire pa nsomba za m'nyanja, ndi pa mbalame za m'mlengalenga, ndi pa zamoyo zonse zakukwawa pa dziko lapansi.
29 Ndipo anati Mulungu, Taonani, ndakupatsani inu therere lonse lakubala mbeu liri pa dziko lapansi, ndi mitengo yonse m'mene muli cipatso ca mtengo wakubala mbeu; cidzakhala cakudya ca inu:
30 ndiponso ndapatsa zinyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za m'mlengalenga, ndi zakukwawa zonse za dziko lapansi m'mene muli moyo, therere laliwisi lonse likhale cakudya: ndipo kunatero.
31 Ndipo anaziona Mulungu zonse zimene adazipanga, ndipo, taonani, zinali zabwino ndithu. Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku lacisanu ndi cimodzi.
1 Ndipo zinatha kupangidwa zakumwamba ndi dziko lapansi, ndi khamu lao lonse.
2 Tsiku lacisanu ndi ciwiri Mulungu anamariza nchito yonse anaipanga; ndipo anapuma tsiku lacisanu ndi ciwiri ku nchito yace yonse.
3 Mulungu ndipo anadalitsa tsiku lacisanu ndi ciwiri, naliyeretsa limenelo: cifukwa limenelo ada puma ku nchito yace yonse imene Mulungu anailenga ndi kupanga.
4 Imeneyo ndiyo mibadwo yao ya zakumwamba ndi dziko lapansi, pamene zinalengedwa, tsiku lomwe Yehova Mulungu anapanga dziko lapansi ndi zakumwamba.
5 Ndi zomera zonse za m'munda zisanakhale m'dziko lapansi, ndiponso matherere onse a m'munda asanamere; cifukwa Yehova Mulungu sanabvumbitsire mvula pa dziko lapansi, ndipo panalibe munthu wakulima nthaka;
6 kama inakwera nkhungu yoturuka pa dziko lapansi, niithirira ponse pamwamba pa nthaka.
7 Ndipo Yehova Mulungu anaumba munthu ndi dothi lapansi, nauzira mpweya wa moyo m'mphuno mwace; munthuyo nakhala wamoyo.
8 Ndipo Yehova Mulungu anabzala m'munda ku Edene cakum'mawa; momwemo ndipo adaika munthu adamuumbayo.
9 Ndipo Yehova Mulungu anameretsa m'nthaka mitengo yonse yokoma m'maso ndi yabwino kudya; ndiponso mtengo wa moyo pakati pa mundapo, ndi mtengo wakudziwitsa zabwino ndi zoipa.
10 Ndipo unaturuka m'Edene mtsinje wakuthirira m'mundamo, m'menemo ndipo unalekana nucita miyendo inai.
11 Dzina la wakuyamba ndi Pisoni: umenewo ndiwo wozungulira dziko lonse la Havila, m'mene muli golidi;
12 golidi wa dziko ali wabwino; ndimonso muli bedola ndi mwala wasohamu.
13 Dzina la mtsinje waciwiri ndi Gihoni: umenewo ndiwo wozungulira dziko lonse la Kusi.
14 Dzina la mtsinje wacitatu ndi Hidikeli: umenewo ndiwo wakuyenda ca kum'mawa kwace kwa Asuri. Mtsinje wacinai ndi Pirate.
15 Ndipo Yehova Mulungu anatenga munthuyo, namuika iye m'munda wa Eriene kuti aulime nauyang'anire.
16 Ndipo Yehova Mulungu anamuuza munthuyo, nati, Mitengo yonse ya m'munda udyeko;
17 koma mtengo wakudziwitsa zabwino ndi zoipa, usadye umenewo; cifukwa tsiku lomwe udzadya umenewo udzafa ndithu.
18 Yehova Mulungu ndipo anati, Si kwabwino kuti munthuakhale yekha; ndidzampangira womthangatira iye.
19 Ndipo Yehova Mulungu anaumba ndi nthaka zamoyo zonse za m'thengo, ndi mbalame zonse za m'mlengalenga; ndipo anapita nazo kwa Adamu kuti aone maina omwe adzazicha; ndipo maina omwe onse anazicha Adamu zamoyo zonse, omwewo ndiwo maina ao.
20 Adamu ndipo anazicha maina zinyama zonse, ndi mbalame za m'mlengalenga ndi zamoyo zonse za m'thengo: koma kwa Adamu sanapezedwa womthangatira iye.
21 Koma Yehova Mulungu anamgonetsa Adamu tulo tatikuru, ndipo anagona: ndipo anatengako nthiti yace imodzi, natsekapo ndi mnofu pamalo pace:
22 ndipo nthitiyo anaicotsa Yehova Mulungu mwa Adamu anaipanga mkazi, ndipo ananka naye kwa Adamu.
23 Ndipo anati Adamu, Uyu tsopano ndiye pfupa la mafupa anga, ndi mnofu wa mnofu wanga; ndipo adzachedwa Mkazi, cifukwa anamtenga mwa mwamuna.
24 Cifukwa cotero mwamuna adzasiya atate wace ndi amace nadzadziphatika kwa mkazi wace: ndipo adzakhala thupi limodzi.
25 Onse awiri ndipo anali amarisece, mwamuna ndi mkazi wace, ndipo analibe manyazi.
1 Ndipo njoka inali yakucenjera yoposa zamoyo zonse za m'thengo zimene anazipanga Yehova Mulungu, Ndipo inati kwa mkaziyo, Ea! kodi anatitu Mulungu, Usadye mitengo yonse ya m'mundamu?
2 Mkaziyo ndipo anati kwa njoka, Zipatso za mitengo ya m'mundamu tidye.
3 Koma zipatso za mtengo umene uti m'kati mwa munda, Mulungu anati, Musadye umenewo, musakhudze umenewo, mungadzafe.
4 Njokayo ndipo inati kwa mkaziyo, Kufa simudzafai;
5 cifukwa adziwa Mulungu kuti tsiku limene mukadya umenewo, adzatseguka maso anu, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wakudziwa zabwino ndi zoipa.
6 Ndipo pamene anaona mkaziyo kuti mtengo unali wabwino kudya, ndi kuti unali wokoma m'maso, mtengo wolakalakika wakupatsa nzeru, anatenga zipatso zace, nadya, napatsanso mwamuna wace amene ali nave, nadya iyenso,
7 Ndipo anatseguka maso ao a onse awiri, nadziwa kuti anali amarisece: ndipo adasoka masamba amkuyu, nadzipangira mateweta.
8 Ndipo anamva mau a Yehova Mulungu alinkuyendayenda m'munda nthawi yamadzulo: ndipo anabisala Adamu ndi mkazi wace pamaso pa Yehova Mulungu pakati pa mitengo ya m'munda.
9 Ndipo Yehova Mulungu anaitana mwamunayo nati kwa iye, Uli kuti?
10 Ndipo anati, Ndinamva mau anu m'mundamu, ndipo ndinaopa cifukwa ndinali wamarisece ine; ndipo ndinabisala.
11 Ndipo anati, Ndani anakuuza iwe kuti uli wamarisece? Kodi wadya za mtengo uja, umene ndinakuuza iwe kuti usadye?
12 Ndipo anati mwamunayo, Mkazi amene munandipatsa ine kuti akhale ndi ine, ameneyo anandipatsa ine za mtengo, ndipo ndinadya.
13 Ndipo Yehova Mulungu anati kwa mkaziyo, Ciani cimene wacitaci? Ndipo anati mkaziyo, Njoka inandinyenga ine, ndipo ndinadya.
14 Ndipo anati Yehova Mulungu kwa njokayo, Cifukwa kuti wacita ici, wotembereredwa ndiwe wopambana ndi zinyama zonse ndi zamoyo zonse za m'thengo: uziyenda ndi pamimba pako, uzidya pfumbi masiku onse a moyo wako:
15 ndipo ndidzaika udani pakati pa iwe ndi mkaziyo, ndi pakati pa mbeu yako ndi mbeu yace; ndipo idzalalira mutu wako, ndipo iwe udzalalira citende cace.
16 Kwa mkaziyo ndipo anati, Ndidzacurukitsa kusauka kwako ndi potenga mimba pako; udzasauka pakubala: udzakhumba mwamuna wako, ndipo iye adzakulamulira iwe.
17 Kwa Adamu ndipo anati, Cifukwa kuti wamvera mau a mkazi wako, nudya za mtengo umene ndinakuuza iwe kuti, Usadyeko; nthaka ikhale yotembereredwa cifukwa ca iwe; m'kusauka udzadyako masiku onse a moyo wako:
18 minga ndi mitula idzakubalira iwe; ndipo udzadya therere la m'thengo:
19 m'thukuta la nkhope yako udzadya cakudya, kufikira kuti udzabwerera kunthaka: cifukwa kuti m'menemo unatengedwa: cifukwa kuti ndiwe pfumbi, ndi kupfumbiko udzabwerera.
20 Ndipo mwamuna anamucha dzina la mkazi wace, Hava; cifukwa ndiye amace wa amoyo onse.
21 Yehova Mulungu ndipo anapangira Adamu ndi mkazi wace maraya azikopa, nawabveka iwo.
22 Ndipo anati Yehova Mulungu, Taonani, munthuyo akhala ngati mmodzi wa ife, wakudziwa zabwino ndi zoipa: ndipo tsopano kuti asatambasule dzanja lace ndi kutenga za mtengo wa moyo, ndi kudya, ndi kukhala ndi moyo nthawi zonse,
23 Yehova Mulungu anamturutsa iye m'munda wa Edene, kuti alime nthaka m'mene anamtenga iye.
24 Ndipo anamuingitsa munthuyo; nakhazika Makerubi ca kum'mawa kwace kwa munda wa Edene, ndi lupanga lamoto lakuzungulira ponsepo, lakusunga njira ya ku mtengo wa moyo.
1 Ndipo mwamunayo anadziwa mkazi wace Hava: ndipo anatenga pakati, nabala Kaini, ndipo anati, Ndalandira munthu kwa Yehova.
2 Ndipo anabalanso mphwace Abele. Abele anakhala mbusa wa nkhosa, koma Kaini anali wakulima nthaka.
3 Ndipo panali atapita masiku, Kaini anatenga zipatso za nthaka, nsembe ya kwa Yehova.
4 Ndiponso Abele anatenga iyenso mwana woyamba wa nkhosa zace ndi mafuta omwe. Yehova ndipo anayang'anira Abele ndi nsembe yace:
5 koma sanayang'anira Kaini ndi nsembe yace. Kaini ndipo anakwiya kwambiri, niigwa nkhope yace.
6 Ndipo Yehova anati kwa Kaini, Ukwiyiranji? Yagweranji nkhope yako?
7 Ukacita zabwino, sudzalandiridwa kodi? Ukaleka kucita zabwino, ucimo ubwatama pakhomo: kwa iwe kudzakhala kulakalaka kwace, ndipo iwe udzamlamulira iye.
8 Kaini ndipo ananena ndi Abele mphwace. Ndipo panali pamene anali kumunda, Kaini anamuukira Abele mphwace, namupha,
9 Yehova ndipo anati kwa Kaini, Ali kuti Abele mphwako? Ndipo anati, Sindidziwai: kodi ndine woyang'anira mphwanga?
10 Ndipo anati, Wacita ciani? Mau a mwazi wa mphwako andipfuulira Ine kunthaka.
11 Tsopano ndiwe wotembereredwa kunthaka, Imene inatsegula pakamwa pace kulandira pa dzanja lako mwazi wa mphwako:
12 pamene udzalima panthaka siidzaperekanso kwa iwe mphamvu yace: udzakhala wothawathawa ndi woyendayenda pa dziko lapansi.
13 Ndipo Kaini anati kwa Yehova, Kulangidwa kwanga nkwakukuru kosapiririka.
14 Taonani, mwandiingitsa ine lero lomwe padziko; ndi pankhope panu ndidzabisika; ndipo ndidzakhala wothawathawa ndi woyendayenda pa dziko lapansi; ndipo kudzatero kuti onse akundipeza adzandipha.
15 Ndipo Yehova anati kwa iye, Cifukwa cace ali yense amene adzapha Kaini kudzabwezedwa kwa iye kasanu ndi kawiri. Ndipo Yehova anaika icizindikiro pa Kaini, kuti asamuphe ali yense akampeza.
16 Ndipo Kaini anaturuka pamaso pa Yehova, ndipo anakhalam'dziko la Nodi, kum'mawa kwace kwa Edene.
17 Ndipo Kaini anamdziwa mkazi wace; ndipo anatenga pakati, nabala Enoke: ndipo anamanga mudzi, naucha dzina lace la mudziwo monga dzina la mwana wace, Enoke.
18 Kwa Enoke ndipo kunabadwa Irade; Irade ndipo anabala Mehuyaeli; Mehuyaeli ndipo anabala Metusaeli; Metusaeli ndipo anabala Lameke.
19 Ndipo Lameke anadzitengera yekha akazi awiri: dzina lace la wina ndi Ada, dzina lace la mnzace ndi Zila.
20 Ndipo Ada anabala Yabala; iye ndiye atate wao wa iwo okhala m'mahema, akuweta ng'ombe,
21 Ndi dzina la mphwace ndilo Yubala; iye ndiye atate wao wa iwo oyimba zeze ndi citoliro.
22 Ndipo Zila, iyenso anabala Tubala-Kaini, mwini wakuphunzitsa amisiri onse a mkuwa ndi a citsulo; mlongo wace wa Tubala-Kaini ndi Nama.
23 Lameke ndipo anati kwa akazi ace: Tamvani mau anga, Ada ndi Zila; Inu akazi a Lameke, mverani kunena kwanga: Ndapha munthu wakundilasa ine, Ndapha mnyamata wakundiphweteka ine,
24 Ngati Kaini adzabwezeredwa kasanu ndi kawiri, Koma Lameke makumi asanu ndi awiri.
25 Ndipo Adamu anadziwanso mkazi wace; ndipo anabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Seti: Cifukwa, nati iye, Mulungu wandilowezera ine mbeu yina m'malo mwa Abele amene Kaini anamupha,
26 Ndiponso kwa Seti, kwa iye kunabadwamwana wamwamuna: anamucha dzina lace Enosi: pomwepo anthu anayamba kuchula dzina la Yehova.
1 Ili ndi buku la mibadwo ya Adamu. Tsiku lomwe Mulungu analenga munthu anamlenga m'cifanizo ca Mulungu;
2 anawalenga iwo mwamuna ndi mkazi, nawadalitsa iwo nacha mtundu wao anthu, tsiku lomwe anawalenga iwo.
3 Ndipo Adamu anakhala ndi moyo zaka zana limodzi kudza makumi atatu, nabala mwana wamwamuna m'cifanizo cace; namucha dzina lace Seti.
4 Masiku ace Adamu atabala Seti, anali zaka mazana asanu ndi atatu; ndipo anabala ana amuna ndi akazi.
5 Masiku ace onse anakhala ndi moyo Adamu anali zaka mazana asanu ndi anai, kudza makumi atatu; ndipo anamwalira.
6 Ndipo Seti anakhala ndi moyo zaka zana kudza zisanu, nabala Enosi;
7 ndipo Seti anakhala ndi moyo, atabala Enosi, zaka mazana asanu ndi atatu kudza zisanu ndi ziwiri: ndipo anabala ana amuna ndi akazi:
8 masiku ace onse a Seti anali zaka mazana asanu ndi anai kudza khumi ndi ziwiri; ndipo anamwalira.
9 Ndipo Enosi anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi anai, nabala Kenani;
10 ndipo anakhala ndi moyo Enosi, atabala Kenani, zaka mazana asanu ndi atatu kudza khumi ndi zisanu: ndipo anabala ana amuna ndi akazi.
11 Masiku ace onse a Enosi anali mazana asanu ndi anai kudza zisanu; ndipo anamwalira.
12 Ndipo Kenani anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi awiri, ndipo anabala Mahalalele:
13 ndipo Kenani anakhala ndi moyo, atabala Mahalalele zaka mazana asanu ndi atatu kudza makumi anai, ndipo anabala ana amuna ndi akazi;
14 masiku ace onse a Kenani anali zaka mazana asanu ndi anai kudza khumi; ndipo anamwalira.
15 Ndipo Mahalalele anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi limodzi kudza zisanu, nabala Yaredi;
16 ndipo Mahalalele anakhala ndi moyo, atabala Yaredi, zaka mazana asanu ndi atatu kudza makumi atatu, nabala ana amuna ndi akazi:
17 masiku ace onse a Mahalalele anali zaka mazana asanu ndi atatu kudza makumi asanu ndi anai ndi zisanu; ndipo anamwalira.
18 Ndipo Yaredi anakhala ndi moyo zaka zana kudza makumi asanu ndi limodzi ndi ziwiri, nabala Enoke;
19 ndipo Yaredi anakhala ndi moyo, atabala Enoke, zaka mazana asanu ndi atatu, nabala ana amuna ndi akazi;
20 masiku ace onse a Yaledi anali zaka mazana asanu ndi anai kudza maitumi asanu ndi limodzi ndi ziwiri: ndipo anamwalira.
21 Ndipo Enoke anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi limodzi kudza zisanu, nabala Metusela:
22 ndipo Enoke anayendabe ndi Mulungu, atabala Metusela, zaka mazana atatu, nabala ana amuna ndi akazi;
23 masiku ace onse a Enoke anali mazana atatu kudza makumi asanu ndi limodzi ndi zisanu;
24 ndipo Enoke anayendabe ndi Mulungu; ndipo panalibe iye; pakuti Mulungu anamtenga.
25 Ndipo Metusela anakhala ndi moyo zaka zana kudza makumi asanu ndi atatu ndi zisanu ndi ziwiri, nabala Lameke;
26 ndipo Metusela anakhala ndi moyo, atabala Lameke, zaka mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu ndi atatu ndi ziwiri, nabala ana amuna ndi akazi:
27 masiku ace onse a Metusela anali mazana asanu ndi anai kudza makumi asanu ndi limodzi kudza zisanu ndi zinai; ndipo anamwalira.
28 Ndipo Lameke anakhala ndi moyo zaka zana kudza makumi asanu ndi atatu ndi ziwiri, nabala mwana wamwamuna;
29 namucha dzina lace Nowa, ndi kuti, Yemweyu adzatonthoza mtima wathu pa nchito zathu zobvuta za manja athu, cifukwa ca nthaka imene anaitemberera Yehova;
30 ndipo Lameke anakhala ndi moyo atabala Nowa, zaka mazana asanu kudza makumi asanu ndi anai ndi zisanu, nabala ana amuna ndi akazi:
31 masiku ace onse a Lameke anali zaka mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu ndi awiri; ndipo anamwa lira.
32 Ndipo Nowa anali wa zaka mazana asanu; ndipo Nowa anabala Semu ndi Hamu ndi Yafeti.
1 Ndipo panali pamene anthu anayamba kucuruka padziko, ndi ana akazi anawabadwira iwo,
2 kuti ana amuna a Mulungu anayang'ana ana akazi a anthu, kuti iwo anali okongola; ndipo anadzitengera okha akazi onse amene anawasankha.
3 Ndipo anati Yehova, Mzimu wanga sudzakangana ndi anthu nthawi zonse, cifukwa iwonso ndiwo thupi lanyama: koma masiku ace adzakhala zaka zana limodzi kudza makumi awiri.
4 Pa dziko lapansi panali anthu akurukuru masiku omwewo ndiponso pambuyo pace, ana amuna a Mulungu atalowa kwa ana akazi a anthu, ndipo anabalira iwo ana, amenewo ndiwo anthu amphamvu akalekale, anthu omveka.
5 Ndipo anaona Yehova kuti kuipa kwa anthu kunali kwakukuru pa dziko lapansi, ndiponso kuti ndingaliro zonse za maganizo a mitima yao zinali zoipabe zokhazokha.
6 Ndipo Yehova anamva cisoni cifukwa anapanga munthu pa dziko lapansi, ndipo anabvutika m'mtima mwace.
7 Ndipo anati Yehova, Ndidzafafaniza anthu amene ndawalenga pa dziko lapansi; anthu, ndi nyama, ndi zokwawa, ndi mbalame za m'mlengalenga: pakuti ndimva cisoni cifukwa ndapanga izo.
8 Koma Nowa anapeza ufulu pamaso pa Yehova.
9 Mibadwoya Nowandiiyi: Nowa anali munthu wolungama ndi wangwiro m'mibadwo yace; Nowa anayendabe ndi Mulungu.
10 Ndipo Nowa anabala ana amuna atatu, Semu, Hamu ndi Yafeti.
11 Ndipo dziko lapansi linabvunda pamaso pa Mulungu, dziko lapansi ndipo linadzala ndi ciwawa.
12 Ndipo Mulungu anaona dziko lapansi, ndipo taonani, linabvunda; pakuti anthu onse anabvunditsa njira yao pa dziko lapansi.
13 Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, Cimariziro cace ca anthu onse cafika pamaso panga; pakuti dziko lapansi ladzala ndi ciwawa cifukwa ca iwo; taonani, ndidzaononga iwo pamodzi ndi dziko lapansi.
14 Udzipangire wekha cingalawa ca mtengo wanjale; upangemo zipinda m'cingalawamo, ndipo upake ndi utoto m'kati ndi kunja.
15 Kupanga kwace ndi kotere: m'litari mwace mwa cingalawa mikono mazana atatu, m'mimba mwace mikono makumi asanu, m'msinkhu mwace mikono makumi atatu.
16 Uike zenera m'ciogalawaco, ulimarize ndi kusiya mkono umodzi pamwamba pace: khomo la cingalawa uike m'mbali mwace; nucipange ndi nyumba yapansi, ndi yaciwiri, ndi yacitatu.
17 Ndine, taonani, ndipo Ine ndidzadzetsa cigumula ca madzi pa dziko lapansi, kuti cionooge zamoyo zonse, m'mene muli mpweya wa moyo pansi pa thambo; zinthu zonse za m'dziko lapansi zidzafa.
18 Koma ndidzakhazikitsa ndi iwe pangano langa; ndipo udzalowa m'cingalawamo iwe ndi ana ako ndi mkazi wako, ndi akazi a ana ako pamodzi ndi iwe.
19 Ndipo zonse zokhala ndi moyo, ziwiri ziwiri za mtundu wao ulowetse m'cingalawamo, kuti zikhale ndi moyo pamodzi ndi iwe; zikhale zamphongo ndi zazikazi.
20 Za mbalame monga mwa mitundu yao, ndi zinyama monga mwa mitundu yao, ndi zokwawa zonse za dziko lapansi monga mwa mitundu yao, ziwiri ziwiri monga mwa mitundu yao, zidzadza kwa iwe kuti zikhale ndi moyo.
21 Ndipo iwe udzitengereko wekha zakudya zonse zodyedwa, oudzisonkhanitsire izi wekha: ndipo zidzakhala zakudya za iwe ndi za iwo.
22 Cotero anacita Nowa, monga mwa zonse anamlamulira iye Mulungu, momwemo anacita.
1 Ndipo anati Yehova kwa Nowa, Talowani, iwe ndi a ku nyumba ako onse m'cingalawamo; cifukwa ndakuona iwe kuti uli wolungama pamaso panga m'mbadwo uno.
2 Nyama zonse zodyedwa udzitengereko wekha zisanu ndi ziwiri, zisanu ndi ziwiri, yamphongo ndi yaikazi yace; ndi nyama zosadyedwa ziwiri ziwiri yamphongo ndi yaikazi yace.
3 Ndiposo mbalame za kumlengalenga zisanu ndi ziwiri, zisanu ndi ziwiri, yaimuna ndi yaikazi, kuti mbeu ikhale ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
4 Pakuti akapita masiku asanu ndi awiri Ine ndidzabvumbitsa mvula pa dziko lapansi masiku makumi anai usana ndi usiku; ndi zinthu zamoyo zonse zomwe ndazipanga ndidzaziononga pa dziko lapansi,
5 Ndipo anacita Nowa monga mwa zonse anamlamulira iye Yehova.
6 Ndipo Nowa anali wa zaka mazana asanu ndi limodzi, pamene cigumula ca madzi cinali pa dziko lapansi.
7 Ndipo analowa Nowa ndi ana ace ndi mkazi wace ndi akazi a ana ace m'cingalawamo, cifukwa ca madzi a cigumula.
8 Nyama zodyedwa ndi nyama zosadyedwa, ndi mbalame, ndi zonse zokwawa pansi,
9 zinalowa ziwiri ziwiri kwa Nowa m'cingalawamo, yamphongo ndi yaikazi, monga momwe Mulungu anamlamulira Nowa.
10 Ndipo panali pamene anapita masiku asanu ndi awiri, madzi a cigumula anali pa dziko lapansi.
11 Caka ca mazana asanu ndi limodzi ca moyo wa Nowa, mwezi waciwiri, tsiku la khumi ndi asanu ndi awiri la mwezi, tsiku lomwelo akasupe onse a madzi akuru anasefuka, ndi mazenera a kumwamba anatseguka.
12 Ndipo mvula inali pa dziko lapansi masiku makumi anai usana ndi usiku.
13 Tsiku lomwelo analowa m'cingalawamo Nowa, ndi Semu, ndi Hamu, ndi Yafeti, ana a Nowa, ndi mkazi wace wa Nowa, ndi akazi atatu a ana ace pamodzi nao:
14 iwo, ndi zamoyo zonse monga mwa mitundu yao, ndi zinyama zonse monga mwa mitundu yao, zokwawa zonse zokwawa pa dziko lapansi monga mwa mitundu yao, ndi zouluka zonse monga mwa mitundu yao, ndi mbalame zonse za mitundu mitundu.
15 Ndipo zinalowa kwa Nowa m'cingalawamo ziwiri ziwiri zamoyo zonse, m'mene muli mpweya wa moyo.
16 Zimene zinalowazo, zinalowa yamphongo ndi yaikazi zamoyo zonse, monga momwe Mulungu anamlamulira iye: ndipo Yehova anamtsekera iye.
17 Ndipo cigumula cinali pa dziko lapansi masiku makumi anai: ndipo madzi anacuruka natukula cingalawa, ndipo cinakwera pamwamba pa dziko lapansi.
18 Ndipo madzi anapambana, nacuruka ndithu pa dziko lapansi, ndipo cingalawa cinayandama pamadzi.
19 Ndipo madzi anapambana ndithu pa dziko lapansi; anamizidwa mapiri atari onse amene anali pansi pa thambo lonse.
20 Madzi anapambana ndithu nakwera mikono khumi ndi isanu: namizidwa mapiri,
21 Ndipo zinafa zamoyo zonse zoyenda pa dziko lapansi, zouluka, ndi nyama, ndi zamoyo, ndi zokwawa zonse zakukwawa pa dziko lapansi, ndi anthu onse:
22 zonse zimene m'mphuno zao munali mpweya wa maimu wa moyo, zonse zinali pamtunda, zinafa.
23 Ndipo zinaonongedwa zamoyo zimene zonse zinali pa dziko lapansi, anthu, ndi nyama, ndi zokwawa, ndi mbalame za m'mlengalenga; ndipo zinaonongedwa pa dzikolapansi: anatsala Nowayekha ndi amene anali pamodzi naye m'cingalawa.
24 Ndipo anapambana madzi pa dziko lapansi masiku zana kudza makumi asanu.
1 Ndipo Mulungu anakumbukira Nowa ndi zamoyo zonse, ndi nyama zonse zimene zinali pamodzi naye m'cingalawamo; ndipo Mulungu anapititsa mphepo pa dziko lapansi, naphwa madzi;
2 ndipo anatsekedwa akasupe a madzi akuru ndi mazenera a kumwamba, niletsedwa mvula ya kwuwamba;
3 ndipo madzi anaphweraphwerabe pa dziko lapansi: pamene anatha masiku zana limodzi kudza makumi atatu madzi anacepa.
4 Ndipo cingalawa cinaima pa mapiri a Ararati, mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku lakhumi ndi asanu ndi awiri la mwezi.
5 Ndipo madzi analinkucepa kufikira mwezi wakhumi; mwezi wakhumi tsiku loyamba mwezi ndipo padaoneka mitu ya mapiri.
6 Ndipo panali atapita masiku makumi anai, Nowa anatsegula pa zenera la cingalawa limene analipanga:
7 ndipo anaturutsa khungubwe, ndipo anaturuka kunka kwina ndi kwina kufikira adaphwa madzi pa dziko lapansi,
8 Ndipo anaturutsa njiwa imcokere, kuti aone kapena madzi anaphwa pamwamba pa dziko lapansi;
9 koma njiwayo siinapeza popondapo phazi lace, nibwera kwa iye kucingalawako, pakuti madzi analipo pa dziko lonse lapansi; ndipo anaturutsa dzanja lace, naitenga, nailowetsa kwa iye m'cingalawamo.
10 Ndipo analinda masiku ena asanu ndi awiri; naturutsanso njiwayo m'cingalawamo;
11 ndipo njiwa inadza kwa iye madzulo; ndipo, taonani, m'kamwa mwace munali tsamba lazitona lotyoledwa: ndipo anadziwa Nowa kuti madzi analimkuphwa pa dziko lapansi.
12 Ndipo analindanso masiku ena asanu ndi awiri; naturutsa njiwayo: ndipo siinabweranso konse kwa iye.
13 Ndipo panali caka ca mazana asanu ndi limodzi kudza cimodzi, mwezi woyamba, tsiku loyamba mwezi, madzi anaphwa pa dziko lapansi; ndipo Nowa anacotsa cindwi lace pacingalawa, nayang'ana, ndipo taonani, padauma pa dziko lapansi.
14 Mwezi waciwiri tsiku la makumi awiri kudza asanu ndi awiri la mwezi, lidauma dziko lapansi.
15 Mulungu ndipo ananena kwa Nowa, kuti,
16 Turukamoni m'cingalawamo, iwe ndi ana ako, ndi mkazi wako, ndi akazi a ana ako pamodzi ndi iwe.
17 Turutsa pamodzi ndi iwe zamoyo zonse ziti ndi iwe za nyama zonse, zouluka, ndi zinyama, ndi zokwawa zonse zakukwawa pa dziko lapansi; kuti ziswane pa dziko lapansi, zibalane, zicuruke pa dziko lapansi.
18 Ndipo anaturuka Nowa ndi ana ace, ndi mkazi wace, ndi akazi a ana ace, pamodzi naye:
19 zinyama zonse, zokwawa zonse, zouluka zonse, ndi zonse zokwawa pa dziko lapansi, monga mwa mitundu yao, zinaturuka m'cingalawamo.
20 Ndipo Nowa anamanga guwa la nsembe la Yehova; natengapo nyama zodyedwa zonse ndi mbalame zodyedwa zonse napereka nsembe zopsereza paguwapo.
21 Ndipo Yehova anamva conunkhira cakukondweretsa; nati Yehova m'mtima mwace, Sindidzatembereranso konse nthaka cifukwa ca munthu; pakuti ndingaliro ya mtima wa munthu iri yoipa kuyambira pa unyamata wace; sindidzaphanso konse zinthu zonse zamoyo, monga momwe ndacitiramo.
22 Pakukhalabe masiku a dziko lapansi, nthawi yakubzala ndi yakukunkha, cisanu ndi mafundi, malimwe ndi msakasa, usana ndi usiku sizidzalekai.
1 Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ace, nati kwa iwo, Mubalane, mucuruke, mudzaze dziko lapansi.
2 Kuopsya kwanu, ndi kucititsa mantha kwanu kudzakhala pa zinyama zonse za dziko lapansi, ndi pa zouluka zonse za m'mlengalenga; ndi pa zonse zokwawa pansi, ndi pa nsomba zonse za m'nyanja, zapatsidwa m'dzanja lanu.
3 Zoyenda zonse zamoyo zidzakhala zakudya zanu; monga therere laliwisi ndakupatsani inu zonsezo.
4 Koma nyama, m'mene muli moyo wace, ndiwo mwazi wace, musadye.
5 Zoonatu mwazi wanu wa miyoyo yanu ndidzafuna; pa dzanja la zinyama zonse ndidzaufuna: ndi pa dzanja la munthu, pa dzanja la mbale wace wa munthu ndidzaufuna moyo wa munthu.
6 Amene akhetsa mwazi wa munthu, ndi munthunso mwazi wace udzakhetsedwa: cifukwa m'cifanizo ca Mulungu Iye anampanga munthu.
7 Ndi inu, mubalane, mucuruke; muswane pa dziko lapansi, nimucuruke m'menemo.
8 Ndipo Mulungu ananena kwa Nowa ndi kwa ana ace pamodzi naye, kuti,
9 Ndipo Ine, taonani, Ine ndikhazikitsa pangano langa pamodzi ndi inu, ndi mbeu zanu pambuyo panu;
10 ndi zamoyo zonse ziti pamodzi ndi inu, zouluka, ng'ombe, ndi zinyama zonse za dziko lapansi, pamodzi ndi inu; zonse zoturuka m'cingalawa, zinyama zonse za dziko lapansi,
11 Ndipo ndidzakhazikitsa pangano langa pamodzi ndi inu; zamoyo zonse sizidzamarizidwanso konse ndi madzi a cigumula; ndipo sikudzakhalanso konse cigumula cakuononga dziko lapansi.
12 Ndipo anati Mulungu, Ici ndici cizindikiro ca pangano limene ndipangana ndi Ine ndi inu, ndi zamoyo zonse ziti pamodzi ndi inu, ku mibadwo mibadwo;
13 ndiika Uta-wa-Leza wanga m'mtambomo, ndipo udzakhala cizindikiro ca pangano lopangana ndi Ine ndi dziko lapansi.
14 Ndipo padzakhala popimba ndi mtambo Ine dziko lapansi, utawo udzaoneka m'mtambomo;
15 ndipo ndidzakumbukira pangano langa limene liri ndi Ine ndi inu, ndi zamoyo zonse zokhala ndi moyo; ndipo madzi sadzakhalanso konse cigumula cakuononga zamoyo zonse.
16 Ndipo utawo udzakhala m'mtambo; ndipo ndidzauyang'anira kuti ndikumbukire pangano lacikhalire liri ndi Mulungu ndi zamoyo zonse zokhala ndi moyo pa dziko lapansi.
17 Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, Ici ndici cizindikiro ca pangano ndalikhazikitsa popaogana ndi Ine ndi zamoyo zonse za pa dziko lapansi.
18 Ndi ana amuna a Nowa amene anaturuka m'cingalawa ndiwo Semu, ndi Hamu, ndi Yafeti: Hamu ndiye atate wace wa Kanani.
19 Amenewa ndiwo ana amuna atatu a Nowa: ndiwo anafalikira dziko lonse lapansi.
20 Ndipo anayamba Nowa kukhala munthu wakulima nthaka, ndipo analima munda wamphesa:
21 namwa vinyo wace, naledzera; ndipo anali wamarisece m'kati mwa bema wace.
22 Ndipo Hamu atate wace wa Kanani, anauona umarisece wa atate wace, nauza abale ace awiri amene anali kunja.
23 Semu ndi Yafeti ndipo anatenga copfunda, naciika pa mapewa ao a onse awiri, nayenda cambuyo, napfunditsa umarisece wa atate wao: nkhope zao zinali cambuyo, osaona umarisece wa atate ao.
24 Nowa ndipo anauka kwa kuledzera kwace, nadziwa cimene anamcitira iye mwana wace wamng'ono.
25 Ndipo anati, Wotembereredwa ndi Kanani: Adzakhala kwa abale ace kapolo wa akapolo:
26 Ndipo anati: Ayamikike Yehova, Mulungu wa Semu; Kanani akhale kapolo wace.
27 Mulungu akuze Yafeti, Akhale iye m'mahema a Semu; Kanani akhale kapolo wace.
28 Ndipo Nowa anakhala ndi moyo cigumula citapita, zaka mazana atatu kudza makumi asanu.
29 Ndipo masiku onse a Nowa anali mazana asanu ndi anai kudza makumi asanu: ndipo anamwalira.
1 Mibadwo ya ana a Nowa, Semu, Hamu, ndi Yafeti, ndi iyi; kwa iwo ndipo kunabadwa ana amuna, citapita cigumula cija.
2 Ana amuna a Yafeti: Gomeri, ndi Magogi, ndi Madai, ndi Yavani, ndi Tubala, ndi Mesheki, ndi Tirasi,
3 Ndi ana amuna a Gomeri: Asekenazo, ndi Rifata, ndi Togarma.
4 Ndi ana amuna a Yavani: Elisa, ndi Tarisisi, ndi Kitimu, ndi Dodanimu.
5 Amenewo ndipo anagawa zisi za amitundu m'maiko mwao, onse amene monga mwa cinenedwe cao; ndi mwa mabanja ao, ndi m'mitundu yao.
6 Ndi ana amuna a Hamu: Kusi, ndi Mizraimu, ndi Puti, ndi Kanani.
7 Ndi ana amuna a Kusi: Seba, ndi Havila, ndi Sabita, ndi Raama, ndi Sabiteka; ndi ana a Raama: Sheba ndi Dedane.
8 Ndipo Kusi anabala Nimrode; ndipo iye anayamba kukhala wamphamvu pa dziko lapansi.
9 Iye ndiye mpalu wamphamvu pamaso pa Yehova: cifukwa cace kunanenedwa, Monga Nimrode mpalu wamphamvu pamaso pa Yehova.
10 Ndipo kuyamba kwace kwa ufumu wace kunali Babele, ndi Ereke, ndi Akadi, ndi Kaline, m'dziko la Sinara.
11 M'dziko momwemo iye anaturuka kunka ku Ashuri, namanga Nineve, ndi mudzi wa Rehoboti, ndi Kala,
12 ndi Resene pakati pa Nineve ndi Kala: umenewo ndi mudzi waukuru.
13 Mizraimu ndipo anabala Ludimu, ndi Anamimu, ndi Lehabimu, ndi Nafituhimu,
14 ndi Patrusimu, ndi Kasiluhimu, m'menemo ndipo anaturuka Afilisti, ndi Kafitorimu.
15 Ndipo Kanani anabala Sidoni woyamba wace, ndi Heti:
16 ndi Ajebusi, ndi Aamori, ndi Agirigasi;
17 ndi Ahivi, ndi Aariki, ndi Asini;
18 ndi Aaravadi, ndi Aazemari, ndi Ahamati; pambuyo pace pamenepo ndipo mabanja a Akanani anafalikira.
19 Ndipo malire a Akanani anayamba pa Sidoni, pakunka ku Gerari ndi ku Gaza; pakunka ku Sodomu, ndi ku Gomora, ndi Adima, ndi Zeboimu, kufikira ku Lasa.
20 Amenewa ndi ana amuna a Hamu monga mwa mabanja ao, mwa zinenedwe zao, m'maiko ao, m'mitundu yao.
21 Ndiponso kwa Semu atate wa ana onse a Ebere, mkuru wa Yafeti, kwa iye kunabadwa ana.
22 Ana amuna a Semu; Elamu, ndi Ashuri, ndi Aripakasadi, ndi Ludi, ndi Aramu.
23 Ndi ana a Aramu: Uzi ndi Huli, ndi Getere, ndi Masi.
24 Aripakasadi ndipo anabala Sela; ndipo Sela anabala Ebere.
25 Kwa Ebere ndipo kunabadwa ana amuna awiri; dzina la wina ndi Pelege; cifukwa kuti m'masiku ace dziko lapansi linagawanikana; dzina la mphwace ndi Yokitani.
26 Ndipo Yokitani anabala Alamodadi, ndi Selefe, ndi Hazaramaveti, ndi Yera;
27 ndi Hadorimu ndi Uzali, ndi Dikila;
28 ndi Obali, ndi Abimaele, ndi Sheva;
29 ndi Ofiri ndi Havila, ndi obabi; onse amenewa ndi ana a okitani.
30 Kwao kunayamba pa Mesa pakunka ku Sefere phiri la kum'mawa.
31 Amenewa ndi ana a Semu, monga mwa mabanja ao, mwa zinenedwe zao, m'maiko ao, m'mitundu yao.
32 Amenewo ndi mabanja a ana a Nowa monga mwa mibadwo yao, m'mitundu yao: ndi amenewo anagawanika mitundu pa dziko lapansi, citapita cigumula.
1 Ndipo dziko lapansi linali la cinenedwe cimodzi ndi cilankhulidwe cimodzi.
2 Ndipo panali pamene anayendayenda ulendo kum'mawa, anapeza cigwa m'dziko la Sinara, ndipo anakhala kumeneko.
3 Ndipo ananenana wina ndi wina, Tiyeni tipange njerwa, tiziocetse. Ndipo anali ndi njerwa naziyesa miyala, ndi katondo anayesa matope.
4 Ndipo anati, Tiyeni, timange mudzi ndi nsanja, pamutu pace pafikire kumwamba; ndipo tidzipangire ife tokha dzina kuti tisabalalike pa dziko lonse lapansi.
5 Ndipo Yehova anatsikira kudzaona mudzi ndi nsanja imene analinkumanga ana a anthu.
6 Ndipo Yehova anati, Taonani, anthu ali amodzi, ndipo onse ali naco cinenedwe cao cimodzi; ndipo ici ayamba kucita: ndipo tsopano palibe kanthu kakuletsedwa nao kamene akafuna kucita.
7 Tiyeni, titsike, pomwepo tisokoneze cinenedwe cao, kuti wina asamvere cinenedwe ca mnzace.
8 Ndipo Yehova anabalalitsa iwo pa dziko lonse lapansi, ndipo analeka kumanga mudzi.
9 Cifukwa cace anacha dzina lace Babele; pakuti kumeneko Yehova anasokoneza cinenedwe ca dziko lonse lapansi; kuyambira pamenepo Yehova anabalalitsa iwo pa dziko lonse lapansi.
10 Mibadwo ya Semu ndi iyi: Semu anali wa zaka zana limodzi ndipo anabala Aripakasadi, citapita cigumula zaka ziwiri;
11 ndipo Semu anakhala ndi moyo zaka mazana asanu, atabala Aripakasadi, nabala ana amuna ndi akazi.
12 Ndipo Aripakasadi anakhala ndi moyo zaka makumi atatu kudza zisanu, nabala Sela;
13 ndipo Aripakasadi anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza zitatu, atabala Sela, nabala ana amuna ndi akazi.
14 Ndipo Sela anakhala ndi moyo zaka makumi atatu, nabala Ebere;
15 ndipo Sela anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza zitatu, atabala Ebere, nabala ana amuna ndi akazi.
16 Ndipo Ebere anakhala ndi moyo zaka makumi atatu kudza zinai, nabala Pelege;
17 ndipo Ebere anakhala ndi moyo zaka mazana anai kudza makumi awiri, atabala Pelege, nabala ana amuna ndi akazi.
18 Ndipo Pelege anakhala ndi moyo zaka makumi atatu, nabala, Reu;
19 ndipo Pelege anakhala ndi moyo zaka mazana awiri kudza zisanu ndi zinai, atabala Reu, nabala ana amuna ndi akazi.
20 Ndipo Reu anakhala ndi moyo zaka makumi atatu kudza ziwiri, nabala Serugi:
21 ndipo Reu anakhala ndi moyo zaka mazana awiri kudza zisanu ndi ziwiri, atabala Serugi, nabala ana amuna ndi akazi.
22 Ndipo Serugi anakhala ndi moyo zaka makumi atatu, nabala Nahori:
23 ndipo Serugi anakhala ndi moyo zaka mazana awiri, atabala Nahori, nabala ana amuna ndi akazi.
24 Ndipo Nahori anakhala ndi moyo zaka makumi awiri kudza zisanu ndi zinai, nabala Tera:
25 ndipo ahori anakhala ndi moyo zaka zana limodzi kudza khumi ndi zisanu ndi zinai, atabala Tera, nabala ana amuna ndi akazi.
26 Ndipo Tera anakhala ndi moyo zaka makumi asanu ndi awiri, nabala Abramu, ndi Nahori ndi Harana.
27 Mibadwo ya Tera ndi iyi: Tera anabala Abramu, ndi Nahori, ndi Harana; ndipo Harana anabala Loti.
28 Ndipo anafa Harana pamaso pa atate wace Tera m'dziko la kubadwa kwace, m'Uri wa kwa Akaldayo.
29 Ndipo Abramu ndi Nahori, anadzitengera okha akazi; dzina lace la mkazi wa Abramu ndilo Sarai; ndi dzina lace la mkazi wa Nahori ndilo Milika, mwana wace wa Harana, atate wace wa Milika, ndi atate wace wa Yisika.
30 Koma Sarai anali wouma; analibe mwana.
31 Ndipo Tera anatenga Abramu mwana wace wamwamuna, ndi Loti mwana wa Harana, mwana wace wamwamuna, ndi Sarai mpongozi wace, mkazi wa mwana wace Abramu; ndipo anaturuka pamodzi nao ku Uri wa kwa Akaldayo kuti amuke ku dziko la Kanani, ndipo anafika ku Harana, nakhala kumeneko.
32 Masiku a Tera anali zaka mazana awiri kudza zisanu; ndipo anafa Tera m'Harana.
1 Ndipo Yehova anati kwa Abramu, Turuka iwe m'dziko lako, ndi kwa abale ako, ndi ku nyumba ya atate wako, kunka ku dziko limene ndidzakusonyeza iwe;
2 ndipo ndidzakuyesa iwe mtundu waukuru, ndipo ndidzakudalitsa iwe, ndi kubukitsa dzina lako; nukhale iwe mdalitso;
3 ndipo ndidzadalitsa amene akudalitsa iwe; ndi kutemberera iye amene akutemberera iwe; ndipo mwa iwe adzadalitsidwa mabanja onse a dziko lapansi,
4 Ndipo anamuka Abramu monga Yehova ananena kwa iye, ndipo Loti anamuka pamodzi naye: ndipo Abramu anali wa zaka makumi asanu ndi awiri kudza zisanu, pamene anaturuka m'Harana.
5 Ndipo Abramu anatenga Sarai mkazi wace, ndi Loti mwana wa mphwace, ndi cuma cao cimene anasonkhanitsa, ndi miyoyo imene anabala m'Harana; naturuka kunka ku dziko la Kanani, ndipo anadza ku dziko la Kanani.
6 Ndipo Abramu anapitira m'dziko kufikira ku malo a Sekemu, kufikira ku mtengo wathundu wa ku More. Akanani anali m'dzikomo nthawi yomweyo.
7 Ndipo Yehova anaonekera kwa Abramu nati, Ndidzapatsa mbeu yako dziko lino: pamenepo anammangira Yehova guwa la nsembe amene anamuonekera iye.
8 Ndipo iye anacoka kumeneko kunka ku phiri la kum'mawa kwa Beteli, namanga hema wace; Beteli anali kumadzulo, ndi Ai anali kum'mawa: kumeneko ndipo anammangira Yehova guwa la nsembe, naitanira dzina la Yehova.
9 Ndipo Abramu anayenda ulendo wace, nayendayenda kunka kumwela.
10 Ndipo munali njala m'dzikomo, ndipo anatsikira Abramo ku Aigupto kukakhala kumeneko, cifukwa kuti njala inali yaikuru m'dziko m'menemo.
11 Ndipo panali pamene anayandikira kulowa m'Aigupto, anati kwa Sarai mkazi wace, Taonani, ndidziwa kuti ndiwe mkazi wokongola maonekedwe ako;
12 ndipo padzakhala pamene adzakuona iwe Aaigupto, adzati, Uyu ndi mkazi wace: ndipo adzandipha ine, koma iwe adzakuleka ndi moyo.
13 Uzikanenatu, kuti iwe ndiwe mlongo wanga: kuti cidzakhala cabwino ndi ine, cifukwa ca iwe, ndi kuti moyo wanga usungike ndi iwe.
14 Ndipo panali pamene Abramu analowa m'Aigupto, Aaigupto anaona kuti mkazi anali wokongola kwambiri.
15 Ndipo akaronga ace a Farao anamuona iye, namyamikira iye kwa Farao; ndipo anamuka ndi mkazi kunyumba kwace kwa Farao.
16 Ndipo anamcitira Abramu bwino cifukwa ca iyeyo; ndipo anali nazo nkhosa, ndi ng'ombe, ndi aburu, ndi akapolo, ndi adzakazi, ndi aburu akazi, ndi ngamila.
17 Koma Yehova anabvutitsa Farao ndi banja lace ndi nthenda zazikuru cifukwa ca Sarai mkazi wace wa Abramu,
18 Ndipo Farao anaitana Abramu, nati, Nanga nciani ici wandicitira ine? cifukwa canji sunandiuza ine kuti ndiye mkazi wako?
19 Cifukwa canji unati, Ndiye mlongo wanga? Kotero ndinamtenga iye akhale mkazi wanga; tsopano suyu mkazi wako; mtenge nucoke.
20 Ndipo Farao analamulira anthu ace za iye; ndipo anamperekeza iye m'njira ndi mkazi wace ndi zonse anali nazo.
1 Ndipo anakwera Abramu kucoka ku Aigupto, iye ndi mkazi wace, ndi zonse anali nazo, ndi Loti pamodzi naye, kunka ku dziko la kumwera.
2 Ndipo Abramu anali wolemera ndithu ndi ng'ombe ndi siliva ndi golidi,
3 Ndipo anankabe ulendowace kucokera ku dziko la kumwera kunka ku Beteli, kufikira kumalo kumene kunali hema wace poyamba paja, pakati pa Beteli ndi Ai;
4 kumalo kwa guwa la nsembe analimanga iye kumeneko, poyamba paja; ndipo pamenepo Abramu anaitanira dzina la Yehova.
5 Ndiponso Loti anayenda ndi Abramu anali ndi nkhosa ndi ng'ombe ndi mahema.
6 Ndipo dziko silinathe kuwakwanira iwo, kuti akhale pamodzi: cifukwa kuti cuma cao cinali cambiri, ndipo sanathe kukhala pamodzi.
7 Ndipo panali ndeu, abusa a Abramu kudana ndi abusa a Loti: Akanani ndi Aperezi ndipo analinkukhala nthawi yomweyo m'dzikomo.
8 Ndipo Abramu anati kwa Loti, Tisacite ndeu, ine ndi iwe, abusa anga ndi abusa ako: cifukwa kuti ife ndife abale.
9 Dziko lonse siliri pamaso pako kodi? Ulekanetu ndi ine: ukanka iwe ku dzanja lamanzere, ine ndinka ku dzanja lamanja: ukanka iwe ku dzanja lamanja, ine ndinka ku dzanja lamanzere.
10 Ndipo Loti anatukula maso ace nayang'ana cigwa conse ca Yordano kuti conseco cinali ndi madzi ambiri, asanaononge Yehova Sodomu ndi Gomora, monga munda wa Yehova, monga dziko la Aigupto pakunka ku Zoari.
11 Ndipo Loti anasankha cigwa conse ca Yordano; ndipo Loti anacoka ulendo wace kunka kum'mawa: ndipo analekana wina ndi mnzace.
12 Ndipo Abramu anakhala m'dziko la Kanani, ndipo Loti anakhala m'midzi ya m'cigwa, nasendeza hema wace kufikira ku Sodomu.
13 Ndipo anthu a ku Sodomu anali oipa ndi ocimwa kwambiri pamaso pa Yehova.
14 Ndipo Yehova anati kwa Abramu, atalekana naye Loti, Tukulatu maso ako, nuyang'anire kuyambira kumene uliko, kumpoto, ndi kumwela, ndi kum'mawa, ndi kumadzulo:
15 cifukwa kuti dziko lonse limene ulinkuona, ndidzakupatsa iwe ndi mbeu yako nthawi yonse.
16 Ndipo ndidzayesa mbeu yako monga pfumbi lapansi: cotere kuti ngati munthu angathe kuwerenga pfumbi lapansi, comweconso mbeu yako idzawerengedwa.
17 Tauka, nuyendeyendc m'dzikoli m'litari mwace ndi m'mimba mwace; cifukwa kuti ndidzakupatsa iwe limenelo.
18 Ndipo Abramu anasuntha hema wace nafika nakhala pa mitengo yathundu ya pa Mamre, imene iri m'Hebroni, nammangira Yehova kumeneko guwa la nsembe.
1 Ndipo panali masiku a Amarafele mfumu ya Sinara, ndi Arioki mfumu ya Elasara, ndi Kedorelaomere mfumu ya Elami, ndi Tidala mfumu ya Goimu,
2 iwo anathira nkhondo pa Bera mfumu ya Sodomu, ndi pa Birisa, mfumu ya Gomora, ndi pa Sinabi mfumu ya Adima, ndi pa Semebere mfumu ya Ziboimu, ndi pa mfumu ya Bela (kumeneko ndi ku Zoari).
3 Onse amenewo anadziphatikana pa cigwa ca Sidimu (pamenepo ndi pa nyanja yamcere).
4 Zaka khumi ndi ziwiri iwo anamtumikira Kedorelaomere, caka cakhumi ndi citatu anapanduka,
5 Caka cakhumi ndicinai ndipo anadza Kedorelaomere ndi mafumu amene anali naye, nawakantha Arefai m'Aseteroti-kamaimu, ndi Azuzi m'Hamu, ndi Aemi m'Savekiriataimu,
6 ndi Ahori pa phiri lao Seiri kufikira ku Eliparana, kumene kuli pacipululu.
7 Ndipo anabwera nafika ku Eni-Misipati (ku meneko ndi ku Kadese), nakantha dziko lonse la Aamaleki, ndiponse Aamori amene akhala m'Hazezoni-tamara.
8 Ndipo anaturuka mfumu ya Sodomu, ndi ya Gomora, ndi mfumu ya Adima, ndi mfumu ya Zeboimu, ndi mfumu ya Bela (kumeneko ndi ku Zoari) ndipo anawathira nkhondo m'cigwa ca Sidimu
9 ndi Kedorelaomere mfumu ya Elamu, ndi Tidala mfumu ya Goimu ndi Amarafele mfumu ya Sinara, ndi Arioki mfumu ya Elasara; mafumu anai kugwirana ndi asanu.
10 Cigwa ca Sidimu cinali ndi zitengetenge tho; ndipo anathawa mafumu a ku Sodomu ndi Gomora nagwa m'menemo: amene anatsala anathawira kuphiri.
11 Ndipo anatenga cuma conse ca Sodomu ndi Gomora ndi zakudya zao zonse, namuka.
12 Ndipo anagwira Loti mwana wa Abramu amene anakhala m'Sodomu, ndi cuma cace, namuka.
13 Ndipo anadza wina amene anapulumuka namuuza Abramu Mhebri; ndipo iye analinkukhala pa mitengo yathundu ya pa Mamre M-amori, mkuru wace wa Esakolo, ndi mkuru wace wa Aneri; amenewo ndiwo opangana naye Abramu.
14 Pamene anamva Abramu kuti mphwace anagwidwa, anaturuka natsogolera anyamata ace opangika, obadwa kunyumba kwace, mazana atatu kudza khumi ndi asanu ndi atatu, nawalondola kutikira ku Dani.
15 Ndipo anadzigawanizira iwo usiku, iye ndi anyamata ace, nawakantha, nawapitikitsa kufikira ku Hoba, ndiko ku dzanja lamanzere la ku Damasiko.
16 Ndipo anabwera naco cuma conse, nabwera naye Loti yemwe ndi cuma cace, ndi akazi ndi anthu omwe.
17 Ndipo anaturuka mfumu ya Sodomu kukomana naye, atabwera anatha kuwakantha Kedorelaomere ndi mafumu amene anali naye, ku cigwa ca Save (ndiko ku cigwa ca mfumu),
18 Ndipo Melikizedeke mfumu ya ku Salemu, anaturuka nao mkate ndi vinyo: iye ndiye wansembe wa Mulungu Wamkurukuru.
19 Ndipo anamdalitsa iye, nati, Abramu adalitsike ndi Mulungu Wamkurukuru, mwini kumwamba ndi dziko lapansi;
20 ayamikike Mulungu Wamkurukuru amene wapereka adani ako m'dzanja lako. Ndipo anampatsa iye limodzi la magawo khumi la zonse.
21 Mfumu ya Sodomu ndipo inati kwa Abramu, Ndipatse ine anthu, nutenge cuma iwe wekha.
22 Ndipo Abramu anati kwa mfumu ya Sodomu, Dzanja langa ndamtukulira Yehova, Mulungu Wamkurukuru, mwini kumwamba ndi dziko lapansi,
23 kuti sindidzatenga ngakhale thonje ngakhale cingwe ca nsapato, ngakhale kanthu kali konse kako, kuti unganene, Ndamlemeza Abramu;
24 koma cokhaci anadya anyamata, ndi gawo lao la anthu amene ananka pamodzi ndi ine, Aneri, Esikolo, ndi Mamre, iwo atenge gawo lao.
1 Zitapita izo, mau a Yehova anadza kwa Abramu m'masomphenya, kuti, Usaope, Abramu, Ine ndine cikopa cako ndi mphotho yako yaikurukuru.
2 Ndipo Abramu anati, Ambuye Mulungu, mudzandipatsa ine ciani popeza ndine wopanda mwana, ndi amene adzakhala mwini nyumba yanga ndiye Eliezere wa ku Damasiko?
3 Ndipo Abramu anati, Taonani, simunandipatse ine mbeu; ndipo, taonani, wobadwa m'nyumba mwanga adzalowa m'malo mwanga.
4 Ndipo, taonani, mau a Yehova anadza kwa iye kuti, Uyu sadzakhala wakulowa m'malo mwako; koma iye amene adzaturuka m'cuuno mwako, ndiye adzakhala wakulowa m'malo mwako.
5 Ndipo anamturutsa iye kunja, nati, Tayang'anatu kumwamba, uwerenge nyenyezi, ngati ukhoza kuziwerenga zimenezo: ndipo anati kwa iye, Zoterezo zidzakhala mbeuzako.
6 Ndipo anakhulupirira Yehova, ndipo kunayesedwa kwa iye cilungamo.
7 Ndipo anatikwaiye, Ine ndine Yehova amene ndinaturutsa iwe m'Uri wa kwa Akaldayo, kuti ndikupatse iwe dziko limeneli likhale lako lako.
8 Ndipo anati, Ambuye Mulungu, nanga ndidzadziwa bwanji kuti lidzakhala colowa canga?
9 Ndipo anati kwa iye, Kanditengere Ine ng'ombe yaikazi ya zaka zitatu, ndi mbuzi yaikazi ya zaka zitatu, ndi tonde wa zaka zitatu, ndi njiwa, ndi bunda.
10 Ndipo anatenga iye zonse zimenezo, nazidula pakati, naika bandu popenyana ndi linzace: koma mbalame sanazidula.
11 Pamene miimba inatsikira panyama, Abramu anaingitsa iyo.
12 Ndipo linalinkulowa dzuwa, ndi tulo tatikuru tinamgwera Abramu: ndipo taonani, kuopsya kwa mdima waukuru kunamgwera iye.
13 Ndipo anati kwa Abramu, Dziwitsa ndithu kuti mbeu zako zidzakhala alendo m'dziko la eni, nizidzatumikira iwo, ndipo iwo adzasautsa izo zaka mazana anai;
14 ndiponso mtunduwo adzautumikira, Ine ndidzauweruza: ndiponso pambuyo pace adzaturuka ndi cuma cambiri.
15 Ndipo iwe udzanka kwa makolo ako m'mtendere; nudzaikidwa ndi ukalambawabwino.
16 Koma iwo adzabweranso kuno mbadwo wacinai: pakuti mphulupulu za Aamori sizinakwaniridwe.
17 Ndipo panali pamene litalowa dzuwa ndi kudza mdima, taonani, ng'anjo yofuka utsi ndi muuni wamoto wapita pakati pa mabanduwo.
18 Tsiku lomwelo Yehova anapangana cipangano ndi Abramu, nati, Ndidzapatsa mbeu zako dziko ili, kuyambira pa nyanja ya Aigupto kufikira pa nyanja yaikuru, nyanja ya Firate:
19 Akeni ndi Akenizi, Akadimoni, ndi Ahiti, ndi Aperezi, ndi Arefai, ndi Aamori, ndi Akanani, ndi Agirigasi, ndi Ajebusi.
1 Ndipo Sarai mkazi wace wa Abramu sanambalire iye mwana; ndipo anali ndi mdzakazi, wa ku Aigupto, dzina lace Hagara.
2 Ndipo Sarai anati kwa Abramu, Taonanitu, Yehova anandiletsa ine kuti ndisabale: lowanitu kwa mdzakazi wanga; kapena ndikalandire ndi iye ana. Ndipo Abramu anamvera mau a Sarai.
3 Ndipo Sarai mkazi wace wa Abramu anatenga Hagara mdzakazi wace wa ku Aigupto, Abramu atakhala m'dziko la Kanani zaka khumi, nampereka iye kwa Abramu mwamuna wace, kuti akhale mkazi wace.
4 Ndipo analowa kwa Hagara, ndipo iye anatenga pakati. Pamene anaona kuti anatenga pakati, anapeputsa wakuka wace m'maso mwace.
5 Ndipo Sarai anati kwa Abramu, Kusauka kwanga kukhale pa iwe: ndakupatsa iwe mdzakazi wanga pamtima pako; ndipo pakuona kuti anatenga pakati anandipeputsa ine m'maso mwace: Yehova aweruze pakati pa iwe ndi ine.
6 Koma Abramu anati kwa Sarai, Taona, mdzakazi wako ali m'dzanja lako, umcitire iye cimene cikukomera m'maso mwako. Ndipo Sarai anamsautsa iye, ndipo anathawa kumaso kwace.
7 Ndipo mthenga wa Yehova anampeza iye pa kasupe wa madzi m'cipululu, pa kasupe wa pa njira ya ku Suri.
8 Ndipo anati, Hagara, mdzakazi wace wa Sarai, ufumira kuti? Unka kuti? Ndipo anati, Ndithawa ine kumaso kwace kwa wakuka wanga Sarai.
9 Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa iye, Bwera kwa wakuka wako, udzicepetse wekha pamanja pace.
10 Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa iye, Ndidzacurukitsa ndithu mbeu zako, kuti unyinji wao sudzawerengeka.
11 Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa iye, Taona, uli ndi pakati, ndipo udzabala mwana wamwamuna; nudzamucha dzina lace Ismayeli; cifukwa Yehova anamva kusauka kwako.
12 Ndipo iye adzakhala munthu wa m'thengo; ndipo dzanja lace lidzakhala lotsutsana ndi anthu onse, ndi manja a anthu onse adzakhala otsutsana naye: ndipo iye adzakhala pamaso pa abale ace onse.
13 Ndipo anacha dzina la Yehova amene ananena naye, Ndinu Mulungu wakundiona ine; pakuti anati, Kodi kunonso ndayang'ana pambuyo pace pa iye amene wakundiona ine?
14 Cifukwa cace citsimeco cinachedwa Beerelahai-roi; taonani ciri pakati pa Kadese ndi Berede.
15 Ndipo Hagara anambalira Abramumwana wamwamuna, ndipo Abramu anacha dzina la mwana wace amene anambalira iye Hagara, lsmayeli.
16 Ndipo Abramu anali wa zaka makumi asanu ndi atatu kudza zisanu ndi cimodzi, pamene Hagara anambalira Abramu Ismayeli.
1 Pamene Abramu anali wa zaka makumi asanu ndi anai kudza zisanu ndi zinai, Yehova anamuonekera Abramu nati kwa iye, Ine ndine Mulungu Wamphamvuyonse; yenda iwe pamaso panga, nukhale wangwiro.
2 Ndipo ndidzapangana pangano langa ndi Ine ndi iwe, ndipo ndidzacurukitsa iwe kwambiri.
3 Ndipo Abramu anagwa nkhope pansi, ndipo Yehova ananena naye kuti,
4 Koma Ine, taona, pangano langa liri ndi iwe, ndipo udzakhala iwe atate wa khamu la mitundu.
5 Sudzachedwanso dzina lako Abramu, koma dzina lako lidzakhala Abrahamu; cifukwa kuti ndakuyesa iwe atate wa khamu la mitundu.
6 Ndipo ndikubalitsa iwe ndithu, ndipo ndidzakuyesa iwe mitundu, ndipo mafumu adzaturuka mwa iwe.
7 Ndipo ndidzalimbitsa pangano langa ndi Ine ndi iwe pa mbeu zako za pambuyo pako m'mibadwo yao, kuti likhale pangano la nthawi zonse, kuti ndikhale Mulungu wako ndi wa mbeu zako za pambuyo pako.
8 Ndipo ndidzakupatsa iwe ndi mbeu zako za pambuyo pako, dziko la maulendo anu, dziko lonse la Kanani likhale lako nthawi zonse: ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wao.
9 Ndipo Mulungu anati kwa Abrahamu, Koma iwe, uzikumbukira pangano langa, iwe ndi mbeu zako za pambuyo pako m'mibadwo yao.
10 Ili ndi pangano langa limene uzisunga pakati pa Ine ndi iwe ndi mbeu zako zapambuyo pako: azidulidwa amuna onse a mwa inu.
11 Muzidula khungu lanu; ndipo cidzakhala cizindikiro ca pangano pakati pa Ine ndi inu.
12 A masiku asanu ndi atatu azidulidwa mwa inu, ana amuna onse m'mibadwo mwanu, amene abadwa m'nyumba ndi amene agulidwa ndi ndalama kwa alendo ali onse, wosakhala mwa mbeu zako.
13 Azidulidwatu amene abadwa m'nyumba mwako ndi amene agulidwa ndi ndalama zako: ndipo pangano langa lidzakhala m'thupi mwako pangano losatha.
14 Ndipo mwamuna wosadulidwa, wosadulidwa khungu lace munthuyo amsadze mwa anthu a mtundu wace; waphwanya pangano langa.
15 Ndipo Mulungu anati kwa Abrahamu, Koma Sarai mkazi wako, usamcha dzina lace Sarai, koma dzina lace ndi Sara.
16 Ndipo ndidzamdalitsa iye, ndiponso ndidzakupatsa iwe mwana wamwamuna wobadwa mwa iye, inde, ndidzamdalitsa iye, ndipo adzakhala amace a mitundu, mafumu a anthu adzaturuka mwa iye.
17 Ndipo Abrahamu adagwa nkhope pansi, naseka, nati m'mtima mwace, Kodi mwana adzabadwa kwa iye amene ali wa zaka zana? Kodi Sara wa zaka makumi asanu ndi anai adzabala?
18 Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, Ha! Ismayeli akhale ndi moyo pamaso panu!
19 Ndipo Mulungu anati, Koma Sara mkazi wako adzakubalira iwe mwana wamwamuna; ndipo udzamucha dzina lace Isake; ndipo ndidzalimbikitsa nave pangano langa, kuti likhale pangano la nthawi zonse, la ku mbeu zace za pambuyo pace.
20 Koma za Ismayeli, ndamvera iwe: taona, ndamdalitsa iye, ndipo ndidzamcurukitsa iye ndithu; adzabala akaronga khumi ndi awiri, ndipo ndidzamuyesa iye mtundu waukuru.
21 Koma pangano langa ndidzalimbikitsa ndi Isake, amene Sara adzakubalira iwe nthawi yomwe yino caka camawa.
22 Ndipo analeka kunena naye, ndipo Mulungu anakwera kucokera kwa Abrahamu.
23 Ndipo Abrahamu anatenga Ismayeli mwana wace ndi onse amene anabadwa m'nyumba mwace, ndi onse, amene anagulidwa ndi ndalama zace, amuna onse a mwa anthu a kunyumba kwace kwa Abrahamu, nadula khungu lao tsiku lomwelo, monga Mulungu ananena naye.
24 Ndipo Abrahamu anali wa zaka makumi asanu ndi anai kudza zisanu ndi zinai, pamene anadulidwa m'khungu lace.
25 Ndipo Ismayeli mwana wace anali wa zaka khumi ndi zitatu pamene anadulidwa m'khungu lace.
26 Tsiku lomwelo anadulidwa Abrahamu ndi Ismayeli mwana wace.
27 Ndipo amuna onse a m'nyumba mwace obadwa m'nyumba, ndi ogulidwa ndi ndalama kwa alendo, anadulidwa pamodzi naye.
1 Ndipo Yehova anamuonekera iye pa mtengo yathundu ya ku Mamre, pamene anakhala pa khomo la hema wace pakutentha dzuwa.
2 Ndipo anatukula maso ace, nayang'ana, taonani, anthu atatu anaima pandunji pace; pamene anaona iwo, anawathamangira kucoka ku khomo la hema kukakomana nao, nawerama pansi, nati,
3 Mbuyanga, ngatitu ndikapeza ufulu pamaso panu, musapitiriretu pa kapolo wanu;
4 nditengetu madzi pang'ono, ndikusambitseni mapazi anu, mupumule pansi pa mtengo;
5 ndipo ndidzatenga cakudya pang'ono, nimutonthoze mitima yanu; mutatero mudzapitirira, cifukwa mwafika kwa kapolo wanu. Ndipo anati, Cita comweco monga momwe wanena.
6 Ndipo Abrahamu analowa msanga m'hema wace kwa Sara, nati, Konza msanga miyeso itatu ya ufa wosalala, nuumbe, nupange mikate.
7 Ndipo Abrahamu anafulumira kunka kuzoweta, natenga kamwana ka ng'ombe kofewa ndi kabwino, napatsa mnyamata, ndipo anafulumira kuphika.
8 Ndipo anatenga mafuta amkaka, ndi mkaka, ndi kamwana ka ng'ombe kamene anaphika, naziika patsogolo pao; ndipo iye anaimirira iwo patsinde pa mtengo, ndipo anadya.
9 Ndipo anati kwa iye, Ali kuti Sara mkazi wako? Ndipo anati, Taonani m'hemamo.
10 Ndipo anati, Ndidzabwera kwa iwe ndithu pakufika nyengo yace; taonani Sara mkazi wako adzakhala ndi mwana wamwamuna. Ndipo Sara anamva pakhomo pa hema amene anali pambuyo pace.
11 Koma Abrahamu ndi Sara anali okalamba, ana pitirira masiku ao; ndipo kunaleka kwa Sara konga kumacita ndi akazi;
12 ndipo Sara anaseka m'mtima mwace, nati, Kodi ndidzakhala ndi kukondwa ine nditakalamba, ndiponso mbuyanga ali wokalamba?
13 Ndipo Yehova anati kwa Abrahamu, Bwanji anaseka Sara, kuti, Kodi ndidzabala ine ndithu, ine amene ndakalamba?
14 Kodi ciripo cinthu comlaka Yehova? Pa nthawi yoikidwa ndidzabwera kwa iwe, pakufika nyengo yace, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.
15 Koma Sara anakana, nati, Sindinasekai; cifukwa anaopa, Ndipo anati, lai; koma unaseka.
16 Ndipo anthuwo anauka kucokera kumeneko nayang'ana ku Sodomu; ndipo Abrahamu ananka nao kuwaperekeza.
17 Ndipo Yehova adati, Kodi ndidzabisira Abrahamu cimene ndicita?
18 Pakuti Abrahamu adzakhala ndithu wamkuru ndi wamphamvu, ndipo mitundu yonse ya dziko lapansi idzadalitsika mwa iye?
19 Cifukwa ndamdziwa iye kuti alamulire ana ace ndi banja lace la pambuyo pace, kuti asunge njira ya Yehova, kucita cilungamo ndi ciweruziro, kuti Yehova akamtengere Abrahamu comwe anamnenera iye.
20 Ndipo anati Yehova, Popeza kulira kwa Sodomu ndi Gomora kuli kwakukuru, ndipo popeza kucimwa kwao kuli kulemera ndithu,
21 ndidzatsikatu ndikaone ngati anacita monse monga kulira kwace kumene kunandifikira: ngati sanatero ndidzadziwa.
22 Ndipo anthuwo anatembenuka nacoka kumeneko, napita kunka ku Sodomu. Koma Abrahamu anaimabe pamaso pa Yehova.
23 Ndipo Abrahamu anayandikira nati, Kodi mudzaononga olungama pamodzi ndi oipa?
24 Kapena alipo olungama makumi asanu m'kati mwa mudzi; kodi mudzaononga, simudzasiya malowa cifukwa ca olungama makumi asanu ali momwemo?
25 Musamatero ai, kupha olungama pamodzi ndi oipa, kuta olungama akhale monga oipa; musamatero ai; kodi sadzacita zoyenera woweruza wa dziko lonse lapansi?
26 Ndipo anati Yehova, Ndikapeza m'Sodomu olungama makumi asanu m'kati mwa mudzi, ndidzasiya malo onse cifukwa ca iwo.
27 Ndipo anayankha Abrahamu nati, Taonanitu, ndadziyesera kunena kwa Ambuye, ine ndine pfumbi ndi phulusa:
28 kapena akaperewera asanu pa olungama makumi asanuwo; kodi mudzaononga mudzi wonse cifukwa ca kuperewera asanu? Ndipo anati, Ndikapeza makumi anai ndi asanu sindidzauononga.
29 Ndipo ananenanso kwa iye nati, Kapena akapezedwa makumi anai m'menemo. Ndipo anati, Sindidzacita cifukwa ca makumi anai.
30 Ndipo anati, Asakwiyetu Ambuye, ndipo ndidzanenanso: kapena akapezedwa makumi atatu m'menemo? Ndipo anati, Ndikapeza makumi atatu m'menemo sindidzacita.
31 Ndipo anati, Taonanitu, ndadziyesera kunena kwa Ambuye: kapena akapezedwa makumi awiri m'menemo. Ndipo anati, Sindidzacita cifukwa ca makumi awiri.
32 Ndipo anati, Asakwiyetu Ambuye, ndipo ndidzanena kamodzi aka kokha: kapena akapezedwakhumim'menemo: Ndipo anati, Sindidzacita cifukwa ca khumi.
33 Ndipo Yehova anapita atatha kunena naye Abrahamu: ndipo Abrahamu anabwera kumalo kwace.
1 Ndipo anadza ku Sodomu madzulo amithenga awiri; ndipo Loti anakhala pa cipata ca Sodomu, ndipo Loti anaona iwo, nauka kuti akakomane nao, ndipo anaweramitsa pansi nkhope yace.
2 Ndipo anati, Taonanitu, ambuye anga, tembenukanitu, kulowa m'nyumba mwa kapolo wanu, mugone usiku wonse, mutsuke mapazi anu, ndipo mudzalawira m'mawa kunka ulendo wanu. Ndipo anati, lai; koma tigone m'khwalalamu usiku wonse.
3 Ndipo anawaumiriza iwo ndithu: ndipo anapatukira kwa iye, nalowa m'nyumba mwace; ndipo anawakonzera iwo madyerero, naphika mikate yopanda cotupitsa, ndipo anadya,
4 Koma asanagone, anthu a m'mudzimo anthu a Sodomu, anazinga nyumba, anyamata ndi okalamba, anthu onse a m'mbali zonse;
5 ndipo anamuitana Loti, nati kwa iye, Ali kuti anthu amene anadza kwa iwe madzulo ano, utiturutsire iwo kuti tiwadziwe.
6 Ndipo Loti anaturukira kwa iwo pakhomo, natseka cambuyo pakhomo pace.
7 Ndipo anati, Abale anga, musacitetu koipa kotere.
8 Taonanitu, ndiri ndi ana akazi awiri, amene sanadziwe mwamuna; ndiwaturutsire iwo kwa inu, mucite nao comwe cikomera inu; koma anthu awa musawacitire iwo kanthu; cifukwa kuti anadza iwo pansi pa mthunzi wa cindwi langa,
9 Ndipo anati iwo, Baima; natinso, Uyu anadza kuno kukhala ngati mlendo, ndipo afuna kutilamulira; tsopano tidzakucitira iwe koipa koposa iwo. Ndipo iwo anamkakamiza munthuyo Loti ndithu, nayandikira kuti aswe citseko.
10 Komo anthu aja anaturutsa dzanja lao, namlowetsa Loti momwe anali iwo m'nyumba, natseka pakhomo,
11 Ndipo anacititsa khungu m'maso mwa anthu amene anali pakhomo pa nyumba, ang'ono ndi akuru, ndipo anabvutika kufufuza pakhomo.
12 Ndipo anthu aja anati kwa Loti, Kodi muli nao ena pano? Mkamwini, ndi ana ako amuna, ndi ana ako akazi, ndi onse ali nao m'mudzi muno, uturuke nao m'malo muno:
13 popeza ife tidzaononga malo ano, cifukwa kulira kwao kwakula pamaso pa Yehova, ndipo Yehova anatitumiza ife kuti tiuononge.
14 Ndipo anaturuka Loti nanena nao akamwini ace amene anakwata ana ace akazi, nati, Taukani, turukani m'malo muno; popeza Yehova adzaononga mudziwu; koma akamwini ace anamyesa wongoseka.
15 Pamene kunaca, amithengawo anafulumiza Loti, nati, Uka, tenga mkazi wako, ndi ana ako akazi awiri amene ali kunowa, kuti munganyeke m'mphulupulu ya mudzi.
16 Koma anacedwa; ndipo anthuwo anamgwira dzanja lace, ndi dzanja la mkazi wace ndi dzanja la ana ace akazi awiri; cifukwa ca kumcitira cifundo Yehova; ndipo anamturutsa iye, namuika kunja kwa mudzi.
17 Ndipo panali pamene anawaturutsa iwo kunja, anati, Tapulumuka ndi moyo wako; usaceuke, usakhale pacigwa pali ponse; thawira kuphiri, kuti unganyeke.
18 Ndipo Loti anati kwa iwo, Iaitu, mfumu;
19 taonanitu, kapolo wanu anapeza ufulu pamaso panu, ndipo munakuza cifundo canu, cimene munandicitira ine, pakupulumutsa moyo wanga; ine sindikhoza kuthawira kuphiri kuti cingandipeze ine coipaco ndingafe:
20 taonanitu, mudzi uwu uli pafupi pothawirapo, ndipo uli wong'ono; ndithawiretu kumeneko, suli wong'ono nanga? ndipo ndidzakhala ndi moyo.
21 Ndipo anati kwa iye, Taona, ndikubvomereza iwe pamenepanso kuti sindidzaononga mudzi uwu umene wandiuza.
22 Fulumira, thawira kumeneko; pakuti sindithai kucita kanthu usadafike kumeneko. Cifukwa cace anacha dzina la mudziwo Zoari.
23 Ndipo dzuwa lidakwera pa dziko pamene Loti anafika ku Zoari.
24 Ndipo Yehova anabvumbitsa pa Sodomu ndi pa Gomora miyala ya sulfure ndi mota kuturuka kwa Mulungu kumwamba;
25 ndipo anaononga midziyo, ndi cigwa conse, ndi onse akukhala m'midzimo, ndi zimene zimera panthaka.
26 Koma mkazi wace anaceuka ali pambuyo pace pa Loti, nasanduka mwala wamcere.
27 Ndipo Abrahamu analawiram'mamawa kunka kumalo kumene anaima pamaso pa Yehova:
28 ndipo anayang'anira ku Sodomu ndi ku Gomora ndi ku dziko lonse la cigwa, ndipo anapenya, taonanitu, utsi wa dzikolo unakwera, monga utsi wa ng'anjo.
29 Ndipo panali pamene Mulungu anaononga midzi ya m'cigwa, Mulungu anakumbukira Abrahamu, naturutsa Loti pakati pa cionongeko, pamene anaononga midzi m'mene anakhalamo Loti.
30 Ndipo Loti anabwera kuturuka m'Zoari nakhala m'phiri ndi ana akazi awiri pamodzi naye: cifukwa anaopa kukhala m'Zoari, ndipo anakhata m'phanga, iye ndi ana ace akazi.
31 Woyamba ndipo anati kwa wamng'ono, Atate wathu akalamba, ndipo palibe pa dziko lapansi mwamona amene adzalowa kwa ife monga amacita pa dziko lonse lapansi:
32 tiyeni, timwetse atate vinyo, tidzagona naye, kuti tisunge mbeu za atate wathu.
33 Ndipo anamwetsa atate wao vinyo usiku womwewo; woyamba ndipo analowa nagona naye atate wace; ndipo sanadziwa pomwe anagona ndi pomwe anauka,
34 Ndipo panali m'mamawa, woyamba anati kwa wamng'ono, Taona, ndinagona ine ndi atate wanga usiku walero: timwetsenso iye usikunso: udzalowe nugone naye kuti tisunge mbeu za atate wathu.
35 Ndipo anamwetsa vinyo atate wao usiku womwenso; wamng'ono ndipo anauka nagona naye; ndipo iye sanadziwa pomwe anagona ndi pomwe anauka.
36 Ndipo ana akazi awiri a Loti anali ndi pakati pa atate wao.
37 Woyamba ndipo anabala mwana wamwamona, namcha dzina lace. Moabu; yemweyo ndi atate wa Amoabu kufikira lero.
38 Wamng'ono ndipo anabala mwana wamwamuna, namcha dzina lace Benammi; yemweyo ndi atate wa Aamoni kufikira lero.
1 Abrahamu ndipo anacoka kumeneko kunka ku dziko la kumwera, ndipo anakhala pakati pa Kedesi ndi Suri, ndipo anakhala ngati mlendo m'Gerari.
2 Ndipo Abrahamu anati za Sara mkazi wace, Iye ndiye mlongo wanga: ndipo Abimeleke mfumu ya Gerari anatumiza namtenga Sara.
3 Koma Mulungu anadza kwa Abimeleke m'kulota kwa usiku, nati kwa iye, Taona, wakufa iwe, cifukwa ca mkazi amene wamtenga: pakuti iye ndiye mkazi wa mwini.
4 Koma Abimeleke sanayandikire naye; ndipo anati, Ambuye, kodi mudzaphanso mtundu wolungama?
5 Kodi iye sanati kwa ine, Ndiye mlongo wanga: ndipo mkazi iye yekha anati, iye ndiye mlongo wanga: ndi mtima wanga wangwiro ndi manja anga osacimwa ndacita ine ici.
6 Ndipo Mulungu anati kwa iye m'kulota, lode ndidziwa ine, kuti wacita ico ndi mtima wangwiro, ndipo lnenso ndinakuletsa iwe kuti usandicimwire ine: cifukwa cace sindinakuloleza iwe kuti umkhudze mkaziyo.
7 Tsopano, umbwezere munthuyo mkazi wace; cifukwa iye ndiye mneneri, ndipo adzakupempherera iwe, ndipo udzakhala ndi moyo: koma ukaleka kumbwezera, udziwe kuti udzafa ndithu, iwe ndi onse amene uli nao.
8 Ndipo Abimeleke analawira m'mamawa, naitana anyamata ace onse, nanena zonse rimenezo m'makutu mwao, ndipo anthu anaopa kwambiri.
9 Ndipo Abimeleke anaitana Abrahamu, nati kwa iye, Waticitira ife ciani iwe? Ndakucimwiranji iwe kuti waufikitsa pa ine ndi pa ufumu wanga ucimo waukuru? Wandicitira ine zosayenera kuzicita.
10 Ndipo Abimeleke anati kwa Abrahamu, Unaona ciani iwe kuti wacita ici?
11 Ndipo Abrahamu anati, Cifukwa ndinati, Pompano palibe ndithu kumuopa Mulungu, ndipo adzandipha ine cifukwa ca mkazi wanga.
12 Koma ndiye mlongo wanga ndithu, mwana wa atate wanga, koma si mwana wa amai wanga: ndipo anakhala ndi ine mkazi wanga.
13 Ndipo panali pamene Mulungu anandiyendetsa ine kunyumba kwa atate wanga, ndinati kwa mkaziyo, Ici ndico cokoma mtima udzandicitire ine, konse kumene tidzafika ife, uzinena za ine, iye ndiye mlongo wanga.
14 Ndipo Abimeleke anatenga nkhosa ndi ng'ombe nd akapolo ndi adzakazi nampatsa Abrahamu, nambwezera iye Sara mkazi wace.
15 Ndipo Abimeleke anati, Taona dziko langa liri pamaso pako; kumene kuli kwabwino pamaso pako takhala kumeneko.
16 Kwa Sara ndipo anati, Taona, ndapatsa mlongo wako ndalama za siliva mazana khumi; taona, izo ndizo zoyeretsa maso za kwa onse amene ali ndi iwe: ndi pamaso pa onse ukhale wolungama.
17 Ndipo Abrahamu anapemphera Mulungu, ndipo Mulungu anaciritsa Abimeleke, ndi mkazi wace, ndi adzakazi ace; ndipo anabala ana.
18 Pakuti Yehova anatseketsa mimba yonse ya a m'nyumba ya Abimeleke, cifukwa ca Sara mkazi wace wa Abrahamu.
1 Ndipo Yehova anayang'anira Sara monga momwe anati, ndipo Yehova anamcitira iye monga ananena.
2 Ndipo Sara anatenga pakati, nambalira Abrahamu m'ukalamba wace mwana wamwamuna, nthawi yomweyo Mulungu anamuuza iye.
3 Ndipo Abrahamu anamucha dzina lace la mwana wace wamwamuna amene anabala iye, amene anambalira iye Sara, Isake.
4 Ndipo Abrahamu anamdula mwana wace wamwamuna Isake pamene anali wa masiku ace asanu ndi atatu, monga Mulungu anamlamulira iye.
5 Ndipo Abrahamu anali wa zaka zana limodzi pamene anambadwira iye Isake mwana wace.
6 Ndipo Sara anati, Mulungu anandisekeretsa ine; onse akumva adzasekera pamodzi ndi ine.
7 Ndipo anati, Akadatero ndani kwa Abrahamu kuti Sara adzayamwitsa ana? pakuti ndambalira iye mwana wamwamuna m'ukalamba wace.
8 Ndipo anakula mwanayo naletsedwa kuyamwa: ndipo Abrahamu anakonza madyerero akuru tsiku lomwe analetsedwa Isake kuyamwa.
9 Ndipo Sara anaona mwana wace wamwamuna wa Hagara M-aigupto, amene anambalira Abrahamu, alinkuseka.
10 Cifukwa cace anati kwa Abrahamu, Cotsa mdzakazi uyo, ndi mwana wace wamwamuna; cifukwa mwana wa mdzakazi uyo sadzalowa m'nyumba pamodzi naye mwana wanga Isake.
11 Ndipo mauwo anaipira Abrahamu cifukwa ca mwana wace.
12 Ndipo Mulungu anati kwa Abrahamu, Usaipidwe nao, cifukwa ca mnyamatayo, ndi cifukwa ca mdzakazi wako; momwe monse akunenera iwe Sara umvere iwe mau ace; cifukwa kuti mwa Isake zidzaitanidwa mbeu zako.
13 Ndipo mwana wamwamuna wa mdzakazi uyo ndidzayesa mtundu, cifukwa iye ndiye mbeu yako.
14 Ndipo Abrahamu analawira m'mamawa, natenga mkate ndi mcenje wa madzi, nampatsa Hagara, naika paphewa pace, ndi mwana, namcotsa iye: ndipo iye anamuka, nasocerera m'cipululu ca Beereseba.
15 Ndipo anatha madzi a m'mcenje ndipo anaika mwana pansi pa citsamba.
16 Ndipo ananka nakhala pansi popenyana naye patari, monga pakugwa mubvi: cifukwa anati, Ndisaone kufa kwa mwana. Ndipo anakhala popenyana naye, nakweza mau ace nalira,
17 Ndipo Mulungu anamva mau a mnyamatayo, ndi mthenga wa Mulungu anamuitana Hagara, ndi mau odzera kumwamba, nati kwa iye, Watani Hagara? usaope; cifukwa Mulungu anamva mau a mnyamata kumene ali.
18 Tauka, nuukitse mnyamatayo, ndi kumgwira m'dzanja lako; cifukwa ndidzamuyesa iye mtundu waukuru.
19 Ndipo Mulungu anamtsegula m'maso mwace, ndipo anaona citsime ca madzi; namuka nadzaza mcenje ndi madzi, nampatsa mnyamata kuti amwe.
20 Ndipo Mulungu anakhala ndi mnyamata, ndipo anakula iye; nakhala m'cipululu, nakhala wauta.
21 Ndipo anakhala m'cipululu ca Parana; ndipo amace anamtengera iye mkazi wa ku dziko la Aigupto.
22 Ndipo panali nthawi yomweyo. Abimeleke ndi Fikolo kazembe wa nkhondo yace anati kwa Abrahamu, kuti, Mulungu ali pamodzi ndi iwe m'zonse uzicita iwe;
23 tsopano iwe undilumbirire ine pano pa Mulungu kuti sudzandinyenga ine, kapena mwana wanga, kapena mdzukulu wanga: koma monga ufulu ndakucitira iwe udzandicitire ine, ndi dziko lomwe wakhalamo, ngati mlendo.
24 Ndipo Abrahamu anati, Ine ndidzalumbira.
25 Ndipo Abrahamu anamdzudzula Abimeleke cifukwa ca citsime ca madzi, anyamata ace a Abimeleke anacilanda.
26 Ndipo anati Abimeleke, Sindinadziwe amene anacita ico; ndipo iwe sunandiuze ine, ndiponso sindinamve koma lero lino.
27 Ndipo Abrahamu anatenga nkhosa ndi ng'ombe, nampatsa Abimeleke, ndipo anapangana pangano onse awiriwo.
28 Ndipo Abrahamu anapatula ana a nkhosa akazi asanu ndi awiri pa okha.
29 Ndipo Abimeleke anati kwa Abrahamu, Nanga ana a nkhosa akazi asanu ndi awiri amene wapatula pa okha?
30 Ndipo anati, Ana a nkhosa akazi asanu ndi awiriwa uwalandire pa dzanja langa, kuti akhale mboni zanga, kuti ndakumba ine citsime cimeneci.
31 Cifukwa cace anacha malowo Beereseba: cifukwa pamenepo analumbira onse awiri.
32 Ndipo anapangana pangano pa Beereseba: ndipo anauka Abimeleke ndi Fikolo kazembe wa-nkhondo yace, nabwera kunka ku dziko la Afilisti.
33 Ndipo Abrahamu ananka mtengo wabwemba pa Beereseba, naitanira pamenepo dzina la Yehova, Mulungu wa nthawi zonse.
34 Ndipo Abrahamu anakhala ngati mlendo masiku ambiri m'dziko la Afilisti.
1 Ndipo panali zitapita zimenezo, Mulungu anamuyesa Abrahamu nati kwa iye, Abrahamu; ndipo anati, Ndine pano.
2 Ndipo anati, Tengatu mwana wako, wamwamuna wayekhayo, Isake, amene ukondana naye, numuke ku dziko la Moriya; numpereke iye kumeneko nsembe yopsereza pa limodzi la mapiri lomwe ndidzakuuza iwe.
3 Ndipo Abrahamu analawira m'mamawa namanga buru wace, natengako anyamata ace awiri pamodzi naye, ndi Isake mwana wace, nawaza nkhuni za nsembe, nauka, nanka kumalo komwe Mulungu anamuuza iye,
4 Tsiku lacitatu Abrahamu anatukula maso ace naona malowo patari.
5 Ndipo Abrahamu anati kwa anyamata ace, Khalani kuno ndi buru, ine ndi mwanayu tinka uko, ndipo tikapemphera ndi kubweranso kwa inu.
6 Ndipo Abrahamu anatenga nkhuni za nsembe yopsereza, nazisenzetsa Isake mwana wace; natenga mota m'dzanja lace ndi mpeni; nayenda pamodzi onse awiri.
7 Ndipo Isake ananena ndi Abrahamu atate wace, nati, Atate wanga; ndipo iye anati, Ndine pano, mwana wanga. Ndipo anati, Taonani moto ndi nkhuni; koma mwana wa nkhosa wa nsembe yopsereza ali kuti?
8 Ndipo Abrahamu anati, Mwana wanga, Mulungu adzadzifunira yekha mwana wa nkhosa wa nsembe yopsereza; nayenda pamodzi onse awiri.
9 Ndipo anafika kumalo komwe Mulungu anamuuza iye; ndipo Abrahamu anamanga guwa la nsembe nakonza nkhuni, namanga Isake mwana wace, namuika iye pa guwa la nsembe pamwamba pa nkhuni.
10 Ndipo Abrahamu anatambasula dzanja lace, natenga mpeni kuti amuphe mwana wace.
11 Koma mthenga wa Yehova anamuitana iye ndi mau odzera kumwamba, nati, Abrahamu, Abrahamu; ndi iye anati, Ndine pano.
12 Ndipo mthenga anati, Usaike dzanja lako pa mwana, usamcitire iye kanthu; cifukwa tsopano ndidziwa kuti iwe umuopa Mulungu, pakuti sunandikanize ine mwana wako, mwana wako wayekha.
13 Ndipo Abrahamu anatukula maso ace nayang'ana taonani, pambuyo pace nkhosa yamphongo yogwiridwa ndi nyanga zace m'ciyangoyangomo; ndipo ananka Abrahamu nakatenga nkhosa yamphongoyo, naipereka nsembe yopsereza m'malo mwa mwana wace.
14 Ndipo Abrahamu anacha dzina lace la malowo Yehova-Yire: monga ati lero lomwe, M'phiri la Yehova cidzaoneka.
15 Ndipo mthenga wa Yehova anamuitana Abrahamu ndi mau odzera kumwamba kaciwiri,
16 nati, Pa Ine ndekha ndalumbira, ati Yehova, popeza wadta ici, sunandikaniza mwana wako, mwana wako wa yekha,
17 kudalitsa ndidzakudalitsa iwe, kucurukitsa ndidzacurukitsa mbeu zako monga nyenyezi za kumwamba, monga mcenga wa m'mphepete mwa nyanja; ndipo mbeu zako zidzagonjetsa cipata ca adani ao;
18 m'mbeu zako mitundu yonse ya dziko lap ansi idzadalitsidwa: cifukwa wamvera mau anga.
19 Ndipo Abrahamu anabwera kwa anyamata ace, ndipo anauka nayenda pamodzi kumuka ku Beereseba; ndipo anakhala Abrahamu pa Beereseba.
20 Ndipo panali zitapita izi, anauza Abrahamu kuti, Taonani, Milika iyenso anambalira Nahori mphwako ana;
21 Huzi woyamba ndi Buzi mphwace, ndi Kemueli atate wace wa Aramu;
22 ndi Kesede, ndi Hazo, ndi Pilidasi ndi Yidilafi, ndi Betuele.
23 Ndimo Betuele anabala Rebeka: amenewa asanu ndi atatu Milika anambalira Nahori mphwace wa Abrahamu.
24 Ndipo mkazi wace wamng'ono, dzina lace Rcuma, iyenso anabala Teba, ndi Gahamu, ndi Tahasi, ndi Maaka.
1 Ndipo Sara anali wa zaka zana limodzi kudza makumi awiri ndi zisanu ndi ziwiri: ndizo zaka za moyo wa Sara.
2 Ndipo Sara anafa m'Kiriyati-araba (ndiwo Hebroni), m'dziko la Kanani; ndipo Abrahamu anadza ku maliro a Sara, kuti amlire.
3 Ndipo Abrahamu anauka pa wakufa wace, nanena kwa ana a Heti, nati,
4 Ine ndine mlendo wakukhala ndi inu: mundipatse ndikhale ndi manda pamodzi ndi inu, kuti ndiike wakufa wanga ndisamthirenso maso.
5 Ndipo ana a Heti anayankha Abrahamu nati kwa iye,
6 Mutimvere ife mfumu, ndinu karonga wamkuru pakati pa ife; muike wakufa wanu m'manda mwathu mosankhika: palibe munthu yense wa ife adzakaniza manda ace, kuti muike wakufa wanu.
7 Ndipo anauka Abrahamu naweramira anthu a m'dzikomo, ana a Heti.
8 Ndipo ananena nao, kuti, Ngati mukandibvomereza kuti ndiike wakufa wanga ndisamthirenso maso, mundimvere ine, mundinenere ine kwa Efroni mwana wace wa Zohari,
9 kuti andipatse ine phanga la Makipela, limene liri pansonga pa munda wace; pa mtengo wace wonse andipatse pakati pa inu, ndikhale nao manda.
10 Ndipo Efroni anakhala pakati pa ana a Heti: ndipo Efroni Mhiti anayankha Abrahamu alinkumva ana a Heti, onse amene analowa pa cipata ca mudzi wace, kuti,
11 Iai, mfumu, mundimvere ine; munda ndikupatsani inu, ndi phanga liri m'menemo ndikupatsani inu, pamaso pa ana a anthu anga ndikupatsani inu; ikani wakufa wanu.
12 Ndipo Abrahamu anawerama pamaso pa anthu a m'dzikomo.
13 Ndipo ananena kwa Efroni alinkumva anthu a m'dzikomo, kuti, Koma ngati ufuna, undimveretu ine: ndidzakupatsa iwe mtengo wace wa munda; uulandire kwa ine, ndipo ndidzaika wakufa wanga m'menemo.
14 Ndipo Efroni anamyankha Abrahamu, nati kwa iye,
15 Mfumu, mundimvere ine; kadziko ka mtengo wace wa masekele a siliva mazana anai, ndiko ciani pakati pa ine ndi inu? ikani wakufa wanu.
16 Ndipo Abrahamu anamvera Effoni, ndipo Abrahamu anamuyesera Efroni ndalama zimene ananena alinkumva ana a Heti, masekele a siliva mazana anai, ndalama zomwezo agulana nazo malonda.
17 Ndipo munda wa Efroni umene unali m'Makipela, umene unali patsogolo pa Mamre, munda ndi phanga liri momwemo, ndi mitengo yonse inali m'mundamo, yokhala m'malire monse mozungulira momwemo,
18 inalimbitsidwa kwa Abrahamu ikhale yace, pamaso pa ana a Heti, pa onse amene analowa pa cipata ca mudzi wace.
19 Zitatha izi Abrahamu anaika Sara mkazi wace m'phanga la munda wa Makipela patsogolo pa Mamre (ndiwo Hebroni), m'dziko la Kanani.
20 Ndipo ana a Heti analimbitsira Abrahamu munda, ndi phanga liri m'menemo, likhale lace lamanda.
1 Ndipo Abrahamu anali wokalamba, nagonera zaka zambiri; ndipo Yehova anadalitsa Abrahamu m'zinthu zonse.
2 Ndipo Abrahamu anati kwa mnyamata wace wamkuru wa pa nyumba yace, amene analamulira pa zonse anali nazo, Taikatu dzanja lako pansi pa ncafu yanga:
3 ndipo ndidzakulumbiritsa iwe pa Yehova, Mulungu wa Kumwamba, ndi Mulungu wa dziko lapansi, kuti usadzamtengere mwana wanga mkazi wa kwa ana akazi a Akananiwo, amene ndikhala pakati pao.
4 Koma udzanke ku dziko langa, kwa abale anga, ndi kumtengera mwana wanga Isake mkazi.
5 Ndipo anati kwa iye mnyamatayo, Kapena sadzafuna mkaziyo kunditsata ine ku dziko lino: kodi ndikambwezerenso mwana wanu kudziko komwe mwacokera inu?
6 Ndipo Abrahamu anati kwa iye, Cenjera iwe, usambwezerenso mwana wanga kumeneko.
7 Yehova Mulungu wa Kumwamba, amene ananditenga ine ku nyumba ya atate wanga, ku dziko la abale anga, amene ananena ndi ine, amene analumbirira ine kuti, Ndidzapatsa mbeu zako dziko ili; iye adzatumiza mthenga wace akutsogolere, ndipo udzamtengere mwana wanga mkazi kumeneko.
8 Ndipo ngati sadzafuna mkaziyo kukutsata iwe, udzakhala wosacimwa pa cilumbiro cangaci: koma mwana wanga usambwezerenso kumeneko.
9 Ndipo mnyamatayo anaika dzanja lace pansi pa ncafu yace ya Abrahamu mbuye wace, namlumbirira iye za cinthuco.
10 Ndipo mnyamatayo anatenga ngamila khumi za mbuyace, namuka: cifukwa kuti cuma conse ca mbuyace cinali m'dzanja lace: ndipo anacoka namuka ku Mesopotamiya, ku mudzi wa Nahori.
11 Ndipo anagwaditsa ngamila zace kunja kwa mudzi, ku citsime ca madzi nthawi yamadzulo, nthawi yoturuka akazi kudzatunga madzi.
12 Ndipo anati, Yehova, Mulungu wa mbuyanga Abrahamu mundiyendetse ine bwino lero lino, mumcitire ufulu mbuyanga Abrahamu,
13 Taonani, ine ndiima pa citsime ca madzi; ndipo ana akazi a m'mudzi aturuka kudzatunga madzi;
14 ndipo pakhale kuti namwali amene ndidzati kwa iye, Tulatu mtsuko wako, ndimwe; ndipo iye adzati, Imwa, ndipo ndidzamwetsanso ngamila zako; yemweyo akhale mkazi wosankhira mnyamata wanu Isake; ndipo cotero ndidzadziwa kuti mwamcitira mbuyanga ufulu.
15 Ndipo panali, asanathe kunena, taonani, anaturuka Rebeka, amene anambala Betuele, mwana wamwamuna wa Milika, mkazi wa Nahori mphwace wa Abrahamu, ndi mtsuko wace paphewa pace.
16 Ndipo namwaliyo anali wokongola kwambiri m'maonekedwe ace, ndiye namwali wosamdziwa mwamuna, ndipo anatsikira kukasupe, nadzaza mtsuko wace, nakwera.
17 Ndipo mnyamatayo anamthamangira kukomana naye, nati, Ndimwetu madzi pang'ono a m'mtsuko mwako.
18 Ndipo anati, Imwa mbuyanga; nafulumira nayangata mtsuko m'manja mwace namwetsa iye.
19 Atatha kumwetsa iye, anati, Ndidzatungiranso ngamila zako, mpaka zitamwa zonse.
20 Ndipo anafulumira nathira madzi a m'mtsuko wace m'comwera, nathamangiranso kucitsime kukatunga, nazitungira ngamila zace zonse.
21 Munthuyo ndipo anamyang'anira iye, nakhala cete, kuti adziwe ngati Yehova anamuyendetsa bwino kapena iai.
22 Ndipo panali zitatha kumwa ngamila, munthuyo anatenga mphete yagolidi ya kulemera kwace sekele latheka, ndi zingwinjiri ziwiri za m'manja ace, kulemera kwace masekele khumi a golidi.
23 Ndipo anati, Ndiwe mwana wa yani? Undiuzetu. Kodi ku nyumba ya atate wako kuli malo akuti tigoneko ife?
24 Ndipo mkaziyo anati kwa iye, Ine ndine mwana wa Betuele mwana wamwamuna wa Milika, amene anambalira Nahori.
25 Natinso kwa iye, Tiri nao maudzu ndi zakudya zambiri oeli malo ogona.
26 Munthuyo oelipo anawerama mutu namyamika Yehova.
27 Ndipo anati, Ayamikike Yehova Mulungu wa mbuyanga Abrahamuamene sanasiya mbuyanga wopanda cifundo cace ndi zoona zace: koma ine Yehova Wanditsogolera m'njira ya ku nyumba ya abale ace a mbuyanga.
28 Namwaliyo ndipo anathamanga nawauza zimenezo ku nyumba ya amace.
29 Ndipo Rebeka anali ndi mlongo wace dzina lace Labani; ndipo Labani anathamangira munthuyo kunja ku kasupe.
30 Ndipo panali, pamene anaona mphete ndi zingwinjiri pa manja a mlongo wace, pamene anamva mau a Rebeka mlongo wace, akuti, Cotero ananena ndi ine munthuyo; Labani anafika pa munthuyo; taonani, anaimirira pa ngamila pakasupe.
31 Ndipo anati, Talowa iwe, wodalitsidwa ndi Yehova; uimiriranji kunjako? cifukwa kuti ndakonzeratu nyumba, ndi malo a ngamila.
32 Munthuyo ndipo analowa m'nyumba, namasula ngamila, napatsa ngamila maudzu ndi cakudya, ndi madzi akusamba mapazi ace ndi mapazi a iwo amene anali naye.
33 Ndipo anaika cakudya pamaso pace: koma anati, Sindidzadya ndisananene cimene ndadzera. Ndipo anati, Nenatu.
34 Ndipo anati, Ine ndine mnyamata wa Abrahamu.
35 Yehova wamdalitsa mbuyanga kwambiri; ndipo anakula kwakukuru; ndipo anampatsa iye nkhosa ndi ng'ombe, ndi siliva ndi golidi, ndi akapolo ndi adzakazi, oeli ngamila ndi aburu.
36 Ndipo Sara mkazi wace wa mbuyanga anambalira mbuyanga mwana wamwamuna, mkaziyo anali wokalamba; ndipo anampatsa mwanayo zonse ali nazo.
37 Ndipo mbuyanga anandilumbiritsa ine kuti, Usamteogere mwana wanga mkazi wa ana akazi a Kanani, m'dziko mwao m'mene ndikhala ine;
38 koma udzanke ku nyumba ya atate wanga, kwa abale anga, ndi kumtengera mwana wanga mkazi.
39 Ndipo ndinati kwa mbuyanga, Kapena mkazi sadzanelitsata ine.
40 Ndipo anati kwa ine, Yehova, amene ndiyenda ine pamaso pace, adzatumiza mthenga wace pamodzi ndi iwe, nadzakuyendetsa bwino m'njira yako; ndipo ukamteogere mwana wanga mkazi wa mwa abale anga ndi ku nyumba ya atate wanga;
41 ukatero udzakhala wosacimwa pa malumbiro ako, pofika iwe kwa abate anga; ndipo ngati sadzakupatsa iwe, udzakhala wosacimwa pa malumbiro ako.
42 Ndipo ndinafika lero kukasupe, ndipo ndinati, Yehova Mulungu wa mbuyanga Abrahamu, ngati mundiyendetsatu bwino njira yanga m'mene ndinkamo ine;
43 taonani, ine ndiima pa kasupe wa madzi, ndipo pakhale, kuti namwali amene aturuka kudzatunga madzi, ndikati kwa iye, Ndipatse madzi ndimwe pang'ono m'mtsuko mwako;
44 ndipo iye akati kwa ine, Imwatu iwe, ndiponso ndidzatungira ngamila zako; yemweyo akhale mkazi amene Yehova wamsankhira mwana wa mbuyanga.
45 Ndisanathe kunena m'mtima mwanga, taonani, Rebeka anaturuka ndi mtsuko wace pa phewa lace, natsikira kukasupe, natunga: ndipo ndinati kwa iye, Ndimwetu.
46 Ndipo iye anafulumira, natsitsa mtsuko pa phewa lace, nati, Imwatu, ndipo ndidzamwetsanso ngamila zako: ndipo ndinamwa, ndipo anamwetsa ngamila.
47 Ndipo ndinamfunsa iye kuti, Ndiwe mwana wa yani kodi? Ndipo anati, Ndine mwana wa Betuele, mwana wa Nahori amene anambalira iye Milika: ndipo ndinaika mphete pamphuno pace ndi zingwinjiri pa manja ace.
48 Ndipo ndinawerama mutu wanga ndi kulambira Yehova, ndi kumyamikira Yehova, Mulungu wa mbuyanga Abrahamu, amene ananditsogolera ine m'njira yakuona, kuti ndikamtengere mwana wamwamuna wace mwana wamkazi wa mphwace wa mbuyanga.
49 Tsopano, ngati mudzamcitira mbuyanga zaufulu ndi zoonadi, mundiuze, ngati iai, mundiuze; kuti ndipatukire ku dzanja lamanja kapena ku dzanja lamanzere.
50 Ndipo anayankha Labani ndi Betuele, nati, Caturuka kwa Yehova cinthu ici; sitingathe kunena ndi iwe coipa kapena cabwino.
51 Taonani, Rebeka ali pamaso pako, mtenge ndi kumuka, akhale mkazi wa mwana wa mbuyako, monga wanena Yehova.
52 Ndipo panali pamene anamva mauwo mnyamata wa Abrahamu, anamgwadira Yehova pansi,
53 Ndipo mnyamatayo anaturutsa zokometsera zasiliva ndi zokometsera zagolidi, ndi zobvala, nampatsa Rebeka: ndipo anapatsa za mtengo wapatari kwa mlongo wace ndi amace.
54 Ndipo anadya namwa iye ndi anthu amene anali pamodzi naye, nagonapo usiku: ndipo anauka m'mamawa, ndipo iye anati, Mundilole ine ndinke kwa mbuyanga.
55 Ndipo mlongo wace ndi amace anati, Namwali akhale ndi ife masiku akuwerengeka, afikire khumi; patsogolo pace iye adzamuka.
56 Ndipo iye anati kwa iwo, Musandicedwetse ine, pakuti Yehova wandiyendetsa bwino m'njira yanga: mundilole ine ndinke kwa mbuyanga.
57 Ndipo anati iwo, Tidzamuitana namwaliyo, tidzamfunsa pakamwa pace.
58 Ndipo anamuitana Rebeka nati kwa iye, Kodi udzanka pamodzi ndi munthuyo? Ndipo anati, Ndidzanka.
59 Ndipo anamlola Rebeka mlongo wao ndi mlezi wace, amuke pamodzi ndi mnyamata wace wa Abrahamu, ndi anthu ace.
60 Ndipo anamdalitsa Rebeka, nati kwa iye, Mlongo wathu ndiwe, iwe ukhale amai wa anthu zikwizikwi, mbeu zako zigonjetse cipata ca iwo akudana nao.
61 Ndipo adauka Rebeka ndi anamwali ace, nakwera pa ngamila natsata munthuyo: mnyamatayo ndipo anamtenga Rebeka namuka.
62 Ndipo Isake anadzera njira ya Beereahai-roi; cifukwa kuti anakhala iye n'dziko la kumwera.
63 Ndipo Isake anaturuka kulingalira m'munda madzulo; ndipo anatukula maso ace, nayang'ana, taona, ngamila zinalinkudza,
64 Ndipo Rebeka anatukula maso ace, ndipo pamene anaonalsake anatsika pa ngamila,
65 Ndipo anati kwa mnyamata, Munthuyo ndani amene ayenda m'munda kukomana ndi ife? Mnyamatayo ndipo anati, Uyo ndi mbuyanga: cifukwa cace namwali anatenga cophimba cace nadziphimba.
66 Mnyamatayo ndipo anamuuza Isake zonse anazicita.
67 Ndipo Isake anamlowetsa mkaziyo m'hema wa amace Sara, namtenga Rebeka, nakhala iye mkazi wace; ndipo anamkonda iye; ndipo Isake anatonthozedwa mtima atafa amace.
1 Ndipo Abrahamu anatenga mkazi wina dzina lace Ketura.
2 Ndipo anambalira iye Zimerani ndi Yokesani ndi Medani, ndi Midyani, ndi Yisebaki, ndi Sua.
3 Ndipo Yokesani anabala Seba, ndi Dedani. Ana a Dedani ndi Aasuri, ndi Aletusi, ndi Aleumi.
4 Ana a Midyani: Efa, ndi Efere, ndi Hanoki, ndi Abida, ndi Elida. Onse amenewa ndi ana a Ketura.
5 Ndipo Abrahamu amwali anampatsa Isake zonse anali nazo.
6 Koma kwa ana a akazi ace ang'ono amene Abrahamu anali nao Abrahamu anapatsa mphatso, nawacotsa iwo kwa Isake mwana wace, akali ndi moyo, kuti anke kum'mawa, ku dziko la kum'mawa.
7 Masiku a zaka za moyo wace wa Abrahamu amene anakhala ndi moyo ndiwo zaka zana limodzi, kudza makumi asanu ndi limodzi, kudza khumi ndi zisanu.
8 Ndipo Abrahamu anamwalira, nafa m'ukalamba wace wabwino, nkhalamba ya zaka zambiri; natengedwa akhale ndi a mtundu wace.
9 Ndipo ana ace Isake ndi Ismayeli anamuika iye m'phanga la Makipela, m'munda wa Efroni mwana wace wa Zohari Mhiti, umene uli patsogolo pa Mamre;
10 munda umene anagula Abrahamu kwa ana a Heti: pamenepo anamuika Abrahamu ndi Sara mkazi wace.
11 Ndipo panali atafa Abrahamu, Mulungu anamdalitsa Isake mwana wace; ndipo Isake anakhala pa Beere-lahai-roi.
12 Mibadwo ya Ismayeli mwana wamwamuna wace wa Abrahamu, amene Hagara M-aigupto mdzakazi wa Sara anambalira Abrahamu ndi iyi:
13 ndipo maina a ana a Ismayeli, maina ao m'mibadwo yao ndi awa: woyamba wa Ismayeli ndi Nebayoti; ndi Kedara, ndi Abideele, ndi Mibisamu,
14 ndi Misima, ndi Duma; ndi Masa;
15 ndi Hadada, ndi Tema, ndi Yeturi, ndi Nafisi, ndi Kedema;
16 ana a Ismayeli ndi awa: maina ao m'midzi yao, m'misasa yao ndi awa: akaronga khumi ndi awiri m'mitundu yao.
17 Zaka za moyo wa Ismayeli ndi izi: zaka zana limodzi kudza makumi atatu ndi zisanu ndi ziwiri: ndipo iye anamwalira, natengedwa akhale ndi a mtundu wace.
18 Ndipo anakhala iwo kuyambira ku Havila kufikira ku Suri, ndiko kum'mawa kwace kwa Aigupto, pakunka ku Asuri: ndipo iye anakhala pamaso pa abale ace onse.
19 Mibadwo ya Isake mwana wace wa Abrahamu ndi iyi: Abrahamu anabala Isake:
20 ndipo Isake anali wa zaka makumi anai pamene anakwata Rebeka, mwana wamkazi wa Betuele Msuriya wa ku Padanaramu, mlongo wace wa Labani Msuriya.
21 Ndipo Isake anampembedzera mkazi wace kwa Yehova popeza anali wouma: ndipo Yehova analola kupembedza kwace, ndipo Rebeka mkazi wace anatenga pakati,
22 Ndipo ana analimbana m'kati mwace: ndipo iye anati, Ngati cotero, ine ndikhala ndi moyo bwanji? ndipo ananka kukafunsa kwa Yehova.
23 Yehova ndipo anati kwa iye, Mitundu iwiri iri m'mimba mwako, Magulu awiri a anthu adzaturuka m'mimba mwako; Gulu lina lidzapambana mphamvu ndi linzace; Wamkuru adzakhala kapolo wa wamng'ono.
24 Atatha masiku ace akubala, taonani, amapasa anali m'mimba mwace.
25 Ndipo woyamba anabadwa wofiira, monse mwace monga maraya aubweya; ndipo anamucha dzina lace Esau.
26 Pambuyo pace ndipo anabadwa mphwace ndipo dzanja lace linagwira citende ca Esau, ndi dzina lace linachedwa Yakobo: ndipo Isake anali wa zaka makumi asanu ndi limodzi pamene mkazi wace anabala iwo.
27 Ndipo anakula anyamatawo; ndipo Esau anali munthu wakudziwa zakusaka nyama, munthu wa m'thengo; ndipo Yakobo anali munthu wofatsa, wakukhala m'mahema.
28 Ndipo Isake anakonda Esau, cifukwa anadya nyama yace ya m'thengo; koma Rebeka anakonda Yakobo,
29 Ndipo Yakobo anaphika mphodza: ndipo Esau anacokera kuthengo, nalefuka:
30 ndipo Esau anati kwa Yakobo, Undipatse ndidye cofiiraco; cifukwa ndalefuka: cifukwa cace anamucha dzina lace Edomu.
31 Ndipo Yakobo anati, Tigulane lero ukulu wako.
32 Ndipo Esau anati, Taona, ine ndifuna kufa: ukuluwo ndidzapindulanii nao?
33 Ndipo anati Yakobo, Undilumbirire ine lero lomwe, ndipo analumbirira iye; nagulana ndi Yakobo ukulu wace.
34 Ndipo Yakobo anampatsa Esau mkate ndi mphodza zophika; ndipo iye anadya, namwa, nanyamuka, napita; comweco Esau ananyoza ukulu wace.
1 Ndipo panali njala padzikopo, yoyenjezeka ndi njala yoyamba ija imene inali masiku a Abrahamu, ndipo Isake ananka kwa Abimeleke mfumu ya Afilisti ku Gerari.
2 Ndipo Yehova anamuonekera iye nati, Usatsikire ku Aigupto, khala m'dziko m'mene ndidzakuuza iwe;
3 khala mlendo m'dziko muno, ndipo Ine ndidzakhala ndi iwe, ndipo ndidzadalitsa iwe cifukwa kuti ndidzakupatsa iwe ndi mbeu zako maiko onse awa, ndipo ndidzalimbikitsa cilumbiriro ndinacilumbirira kwa Abrahamu atate wako;
4 ndipo ndidzacurukitsa mbeu zako monga nyenyezi za kumwamba, ndipo ndidzapatsa mbeu zako maiko onsewa; m'mbeu zako mitundu yonse ya dziko lapansi idzadalitsidwa;
5 cifukwa kuti Abrahamu anamvera mau anga, nasunga cilangizo canga, ndi maweruziro anga, ndi malemba anga ndi malamulo anga.
6 Ndipo Isake anakhala m'Gerari;
7 ndipo anthu a kumeneko anamfunsa iye za mkazi wace; ndipo iye anati, diye mlongowanga: cifukwa kuti anaopa kunena, Mkazi wanga; anati, anthu a kumeneko angandiphe ine cifukwa ca Rebeka; popeza anali wokongola pakumuona.
8 Ndipo panali atakhala komwe masiku ambiri, Abimeleke mfumu ya Afilisti, anayang'ana kunja kwa zenera, napenya, taona, Isake analinkuseka ndi Rebeka mkazi wace.
9 Ndipo Abimeleke anamuitana Isake nati, Taona, uyo ndi mkazi wako ndithu: kodi bwanji unati, Ndiye mlongo wanga? Ndipo Isake anati kwa iye, Cifukwa ndinati, Ndingafe cifukwa ca iye.
10 Ndipo Abimeleke anati, Nciani cimeneci waticitira ife? panatsala pang'ono ena a anthu akadagona naye mkazi wako, ndipo ukadaticimwitsa ife:
11 Ndipo Abimeleke anauza anthu ace, nati, Ali yense amene akhudza mwamuna uyo kapena mkazi wace, zoonatu adzaphedwa.
12 Ndipo Isake anabzala m'dzikomo, nalandira za makumi khumi caka cimeneco; ndipo Yehova anamdalitsa iye.
13 Ndipo anakula munthuyo, nakulakula kufikira kuti anakhala wamkurukuru:
14 ndipo anali ndi cuma ca nkhosa, ndi cuma ca zoweta, ndi banja lalikuru: ndipo Afilisti anamcitira iye nsanje.
15 Ndipo zitsime zonse anakumba anyamata a atate wace Afilisti anazitseka, nazikwirira ndi dothi.
16 Ndipo Abimeleke anati kwa Isake, Ucoke kwa ife cifukwa kuti iwe uti wamkuru wopambana ife.
17 Ndipo Isake anacoka kumeneko, namanga hema wace m'cigwa ca Gerari, nakhala kumeneko.
18 Ndipo Isake anafukulanso zitsime za madzi, anazikumba masiku a Abrahamu atate wace; cifukwa kuti Afilisti anazitseka atafa Abrahamu: ndipo anazicha maina monga maina omwe anazicha atate wace.
19 Ndipo anyamata a Isake anakumba m'cigwa, napeza kumeneko citsime ca madzi otumphuka.
20 Ndipo abusa a Gerari anakangana ndi abusa a Isake kuti, Madzi ndi athu; ndipo anacha dzina la citsimeco Eseke: cifukwa anakangana nave.
21 Ndipo anakumbanso citsime cina, ndipo anakangana naconso; nacha dzina lace Sitina.
22 Ndipo anacoka kumeneko nakumba citsime cina; koma sanakangana naco cimeneco; ndipo anacha dzina lace Rehoboti; ndipo anati, Cifukwa kuti tsopano Yehova anatipatsa ife malo, ndipo tidzabalana m'dziko muno.
23 Ndipo anacoka kumeneko nakwera kunka ku Beereseba,
24 Ndipo Yehova anamuonekera iye usiku womwewo, nati, Ine dine Mulungu wa Abrahamu atate wako; usaope, cifukwa kuti Ine ndiri ndi iwe, ndipo ndidzakudalitsa iwe, ndi kucurukitsa mbeu zako, cifukwa ca Abrahamu kapolo wanga.
25 Ndipo anamanga kumeneko guwa la nsembe, naitana dzina la Yehova, namanga hema wace kumeneko: ndi pamenepo anyamata a Isake anakumba citsime.
26 Ndipo ananka kwa iye Abimeleke kucokera ku Gerari, ndi Ahuzati bwenzi lace, ndi Fikoli, kazembe wa nkhondo yace.
27 Ndipo Isake anati kwa iwo, Mwandidzera cifukwa ciani, inu akundida ine, ndi kundicotsa kwanu?
28 Ndipo iwo anati, Kuona tinaona kuti Yehova ali ndi iwe; ndipo tinati, Tilumbiriranetu tonse awiri, ife ndi iwe, ticite pangano ndi iwe;
29 kuti usaticitire ife zoipa, pakuti sitidakhudza iwe, sitidakucirira kanthu koma kabwino ndiko, ndipo takulola umuke ndi mtendere; ndiwe tsopano wodalitsidwa ndi Yehova.
30 Ndipo anakonzera iwo madyerero, ndipo anadya namwa.
31 Ndipo analawira m'mamawa nalumbirirana wina ndi mnzace; ndipo Isake anawalola amuke, ndipo anauka kucokera kwa iye m'mtendere.
32 Ndipo panali tsiku lomwelo anyamata ace a Isake anadza namuuza iye za citsime cimene anakumba, nati kwa iye, Tapeza madzi.
33 Ndipo anacha dzina lace Seba, cifukwa cace dzina la mudziwo ndi Beereseba kufikira lero lino.
34 Pamene Esau anali wa zaka makumi anai, anakwatira Yuditi mwana wamkazi wa Beeri Mhiti, ndi Basemati mwana wamkazi wa Elone Mhiti:
35 ndipo iwo anapweteka mtima wa Isake ndi wa Rebeka.
1 Ndipo panali atakalamba Isake, ndi maso ace anali a khungu losaona nalo, anamuitana Esau mwana wace wamwamuna wamkuru, nati kwa iye, Mwana wanga; ndipo anati kwa iye, Ndine pano.
2 Ndipo anati, Taonatu, ndakalamba, sindidziwa tsiku la kufa kwanga:
3 tsopano tengatu zida zako ndi phodo lako ndi uta wako, numuke kuthengo kundisakira ine nyama;
4 nundikonzere ine cakudya cokolera conga comwe ndicikonda ine, nudze naco kwa ine kuti ndidzadye; kuti moyo wanga ukadalitse iwe ndisanafe.
5 Ndipo anamva Rebeka pamene Isake ananena ndi Esau mwana wace. Ndipo Esau ananka kuthengo kukasaka nyama ndi kubwera nayo.
6 Ndipo Rebeka ananena kwa Yakobo mwana wace, nati, Taona ndinamva atate wako alinkunena ndi Esau mkuru wako kuti,
7 Unditengere ine nyama, undikonzere ine cakudya cokolera, kuti ndidzadye, ndi kudalitsa iwe pamaso pa Yehova, ndisanafe.
8 Tsopanotu mwana wanga, tamvera mau anga monga momwe nditi ndikuuze iwe.
9 Pitatu kubusa, ukanditengere ine kumeneko tiana tiwiri tabwino ta mbuzi; ndikonzere nato cakudya cokolera ca atate wako conga comwe acikonda:
10 ndipo udzapita naco kwa atate wako, kuti adye, ndi kukudalitsa iwe asanafe,
11 Yakobo ndipo anati kwa Rebeka amace, Taonani, Esau mkuru wanga ndiye munthu waubweya, ine ndine munthu, wosalala.
12 Kapena atate wanga adzandiyambasa, ndipo ndidzaoneka pamaso pace ngati wakunyenga; pamenepo ndidzadzitengera ine temberero, si mdalitso.
13 Ndipo amace anati kwa iye, Pa ine likhale temberero lako mwana wanga; koma tamvera mau anga, kazimuka kunditengera timeneto.
14 Ndipo anamuka nakatenga nadza nato kwa amace; amace ndipo anakonza cakudya cokolera conga cimene anacikonda atate wace.
15 Ndipo Rebeka anatenga zobvala zokoma za Esau, mwana wace wamkuru zinali m'nyumba, nabveka nazo Yakobo mwana wace wamng'ono;
16 ndipo anabveka zikopa za tiana tambuzi pa manja ace ndi pakhosi pace posalala;
17 ndipo anapereka m'dzanja la mwana wace Yakobo cakudya cokoleraco, ndi mikate imene anaipanga.
18 Ndipo iye analowa kwa atate wace, nati, Atate wanga; iye anati, Ndine pano; ndani iwe mwana wanga?
19 Ndipo Yakobo anati kwa atate wace, Ndine Esau mwana wanu wamkuru; ndacita monga mwandiuza ine; ukanitu, khalani tsonga, idyani nyama yanga kuti moyo wanu undidalitse ine.
20 Ndipo Isake anati kwa mwana wace, Unaipeza msanga bwanji mwana wanga? Ndipo anati, Cifukwa kuti Yehova Mulungu wanu anandiyendetsa ine bwino.
21 Ndipo Isake anati kwa Yakobo, Sendera kuno, ndikuyambase mwana wanga, ngati ndiwe mwana wanga Esau ndithu, kapena wina.
22 Ndipo Yakobo anasendera kwa Isake atate wace, ndipo anamyambasa nati, Mau ndi mau a Yakobo, koma manja ndi manja a Esau.
23 Ndipo sanazindikira iye, cifukwa kuti manja ace anali aubweya, onga manja a Esau mkuru wace; ndipo anamdalitsa iye.
24 Ndipo anati, Kodi ndiwe mwana wanga weniweni Esau? ndipo anati, Ndine amene.
25 Ndipo iye anati, Usendere nayo kwa ine, ndidye nyama ya mwana wanga, kuti moyo wanga ukudalitse iwe. Ndipo anasendera nayo kwa iye, nadya iye; ndipo anamtengera vinyo, namwa iye.
26 Ndipo Isake atate wace anati kwa iye, Senderatu, undimpsompsone mwana wanga.
27 Ndipo anasendera nampsompsona; ndipo anamva kununkhira kwa zobvala zace, namdalitsa, nati, Taona, kununkhira kwa mwana wanga, Kufanana ndi kununkhira kwa munda anaudalitsa Yehova;
28 Mlungu akupatse iwe mame a kumwamba, Ndi zonenepa za dziko lapansi, Ndi tirigu wambiri ndi vinyo;
29 Anthu akutumikire iwe, Mitundu ikuweramire iwe; Ucite ufumu pa abale ako, Ana a amako akuweramire iwe; Wotemberereka ali yense akutemberera iwe, Wodalitsika ali yense akudalitsa iwe.
30 Ndipo panali atatha Isake kumdalitsa Yakobo, ataturuka Yakobo pamaso pa Isake atate wace, Esau mkuru wace analowa kucokera kuthengo,
31 Ndipo iyenso anakonza cakudya cokolera, nadza naco kwa atate wace, nati kwa atate wace, Auke atate wanga, adye nyama ya mwana wace, kuti moyo wanu undidalitse ine.
32 Ndipo Isake atate wace anati kwa iye, Ndiwe yani? ndipo iye anati, Ndine mwana wanu woyamba Esau.
33 Ndipo Isake ananthunthumira ndi kunthunthumira kwakukuru, nati, Ndani uja anatenga nyama, nadza nayo kwa ine, ndipo ndadyako zonse usadaloweiwe, ndipondamdalitsaiye? inde, adzadalitsika.
34 Pamene Esau anamva mau a atate wace Isake, analira ndi kulira kwakukuru ndi kowawa kopambana, nati kwa atate wace, Mundidalitse ine, inenso atate wanga.
35 Ndipo iye anati, Mphwako anadza monyenga, nalanda mdalitso wako.
36 Ndipo iye anati, Kodi si ndico cifukwa anamucha dzina lace Yakobo? kuti wandinyenga ine kawiri aka; analanda ukulu wanga ndipo taonani, tsopano walanda mdalitso wanga. Ndipo anati, Kodi smunandisungira ine mdalitso?
37 Ndipo anayankha Isake nati kwa Esau, paona, ndamuyesa iye mkuru wako, ndi abale ace onse ndampatsa iye akhale akapolo ace; ndakhazikitsa iye ndi tirigu ndi vinyo; nanga pamenepo mwana wanga, ndidzakucitira iwe ciani?
38 Ndipo Esau anati kwa atate wace, Kodi muli nao mdalitso umodzi wokha, atate wanga? Mundidalitse ine, inenso, atate wanga, Ndipo Esau anakweza mau ace nalira.
39 Ndipo Isake atate wace anayankha nati kwa iye, Taona, pokhala pako mpa zonenepa za dziko lapansi, Mpa mame a kumwamba akudzera komwe;
40 Udzakhala ndi moyo ndi lupanga lako, nudzakhala kapolo wamphwako; Ndipo padzakhalapamene udzapulumuka, Udzacotsa gori lace pakhosi pako.
41 Ndipo Esau anamuda Yakobo cifukwa ca mdalitso umene atate wace anamdalitsa nao: ndipo Esau anati m'mtima mwace, Masiku a maliro a atate wanga ayandikira; pamenepo ndipo ndidzamupha mphwanga Yakobo.
42 Ndipo anauza Rebeka mau a Esau mwana wace wamkuru: ndipo iye anatumiza naitana Yakobo mwana wace wamng'ono, nati kwa iye, Taona, mkuru wako Esau, kunena za iwe, adzitonthoza yekha mtima wace kuti adzakupha iwe.
43 Ndipo tsopane mwana wanga, tamvera mau anga: tauka, nuthawire kwa Labani mlongo wanga ku Harana;
44 ukhale naye masiku akuwerengeka, mpaka wamcokera ukali wa mkuru wako;
45 mpaka wakucokera mkwiyo wa mkuru wako, kuti aiwale cimene wamcitira iye; pamenepo ndipo ndidzatumiza kukutenganso iwe kumeneko; ndidzakhala bwanji wopanda inu nonse awiri tsiku limodzi?
46 Ndipo anati Rebeka kwa Isake, Ndalema moyo wanga cifukwa ca aria akazi a Heti: akatenga Yakobo mkazi wa ana akazi a Heti, onga ana akazi a m'dziko lino, moyo wanga udzandikhalira ine bwanji?
1 Ndipo Isake anamuitana Yakobo, namdalitsa iye, namuuza iye, nati kwa iye, Usatenge mkazi wa ana akazi a Kanani.
2 Tauka, nupite ku Padanaramu, ku nyumba ya Betuele, atate wa amai ako; ukadzitengere mkazi wa kumeneko kwa ana akazi a Labani mlongo wace wa amako.
3 Mulungu Wamphamvuyonse akudalitse iwe, akubalitse iwe, akucurukitse iwe, kuti ukhale khamu la anthu:
4 akupatse iwe mdalitso wa Abrahamu, iwe ndi mbeu zako pamodzi nawe: kuti ulowe m'dziko limene ukhalamo mlendo, limene Mulungu anampatsa Abrahamu.
5 Ndipo Isake anamlola Yakobo amuke, ndipo ananka ku Padanaramu kwa Labani, mwana wace wa Betuele Msuriya, mlongo wace wa Rebeka, amai wao wa Yakobo ndi Esau.
6 Ndipo anaona Esau kuti Isake anamdalitsa Yakobo namtumiza ku Padanaramu kuti atenge mkazi wa kumeneko;
7 ndiponso kuti pamene anamdalitsa iye, anamuuza iye kuti, Usatenge mkazi wa ana akazi a Kanani; ndiponso kuti Yakobo anamvera atate wace ndi amace, nanka ku Padanaramu;
8 ndipo Esau anaona kuti ana akazi a Kanani sanakondweretsa Isake atate wace:
9 ndipo ananka kwa Ismayeli, naonjezera kwa akazi amene anali nao, natenga Mahalati mwana wamkazi wa Ismayeli mwana wa Abrahamu, mlongo wace wa Nebayoti akhalemkazi wace.
10 Ndipo Yakobo anacoka m'Beereseba, nanka ku Harana.
11 Ndipo anafika kumalo, nagona kumeneko usiku, cifukwa lidalowa dzuwa: ndipo anatenga mwala wa kumeneko, nauika pansi pa mutu wace, nagona tulo kumeneko.
12 Ndipo analota, taonani, makwerero anaima pansi, pamwamba pace ndipo padafikira kumwamba: ndipo, taonani, amithenga a Mulungu analinkukwera, analinkutsika pamenepo.
13 Taonani, Yehova anaima pamwamba pace, nati, Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu atate wako, ndi Mulungu wa Isake; dziko limene ulinkugonamo ndidzakupatsa Iwe ndi mbeu zako;
14 mbeu zako zidzakhala monga pfumbi lapansi, ndipo udzabalalikira kumadzulo ndi kum'mawa ndi kumpoto ndi kumwera: mwa iwe ndi mu mbeu zako mabanja onse a dziko lapansi adzadalitsidwa.
15 Taonani, Ine ndiri pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakusunga iwe konse kumene upitako, ndipo ndidzakubwezanso iwe ku dziko lino; cifukwa kuti sindidzakusiya iwe, kufikira kuti nditacita cimene ndanena nawe.
16 Ndipo Yakobo anauka m'tulo tace, nati, Ndithu, Yehova ali mommuno; ndipo sindinadziwe.
17 Ndipo anaopa, nati, Poopsya pompano! pompano ndipo pa nyumba ya Mulunga, si penai, pompano ndipo pa cipata ca kumwamba.
18 Yakobo ndipo anauka m'mamawa, natenga mwala umene anaika pansi pa mutu wace, nauimiritsa, nathira mafuta pamtu pace.
19 Ndipo anacha dzina la pamenepo Beteli; pakuyamba dzina lace la mudziwo ndi Luzi.
20 Yakobo ndipo analumbiracilumbiro, nati, Mulungu akakhala ndi ine, akandisunga ine m'njira imene ndipitamo, akandipatsa ine mkate wa kudya, ndi zobvalira za kubvala,
21 kuti ndibwerenso ku nyumba ya atate wanga ndi mtendere, pamenepo Yehova adzakhala Mulungu wanga,
22 ndi mwala umenewu ndinauimiritsa, udzakhala nyumba ya Mulungu; ndipo la zonse mudzandipatsa ine, ndidzakupatsani Inu limodzi la magawo khumi.
1 Ndipo Yakobo ananka ulendo wace, nafika ku dziko la anthu a kum'mawa.
2 Ndipo anayang'ana, taonani, citsime m'dambo, ndipo, taonani, magulu atatu a nkhosa alinkugona kumeneko: pakuti pacitsimepo anamwetsa nkhosa; ndipo mwala wa pakamwa pa citsime unali waukuru.
3 Kumeneko ndipo zinasonkhana zoweta zonse: ndipo anagubuduza mwala kuucotsa pakamwa pa citsime, namwetsa nkhosa, naikanso mwala pakamwa pa citsime pamalo pace.
4 Ndipo anati Yakobo kwa iwo, Abale anga, ndinu a kuti inu? nati, Ndife a ku Harana.
5 Ndipo anati kwa iwo, Kodi mumdziwa Labani mwana wace wa Nahori? nati, Timdziwa.
6 Ndipo anati kwa iwo, Kodi ali bwino? nati, Ali bwino: taonani, Rakele mwana wace wamkazi alinkudza nazo nkhosa.
7 Ndipo iye anati, Taonani, kukali msana, si nthawi yosonkhanitsa zoweta; mwetsani nkhosa, pitani, kadyetseni.
8 Ndipo anati, Sitingathe, koma zitasonkhana ziweto zonse, ndipo atagubuduza mwala kuucotsa pakamwa pa citsime ndiko; pamenepo ndipo tizimwetsa nkhosa.
9 Ali cilankhulire nao, anafika Rakele ndi nkhosa za atate wace, cifukwa anaziweta.
10 Ndipo panali pamene Yakobo anaona Rakele, mwana wamkazi wa Labani, mlongo wace wa amace, ndi nkhosa za Labani mlongo wace wa amace, Yakobo anayandikira nagubuduza kuucotsa mwala pacitsime, nazimwetsa zoweta za Labani, mlongo wace wa amace.
11 Ndipo Yakobo anampsompsona Rakele nakweza mau ace, nalira.
12 Ndipo Yakobo anamuuza Rakele kuti iye ndiye mbalewace wa atate wace, kuti ndiye mwana wace wa Rebeka, ndipo Rakele anathamanga nakauza atate wace.
13 Ndipo panali pamene Labani anamva mbiri ya Yakobo mwana wa mlongo wace, iye anathamangira kukakomana naye namfungatira, nampsompsona, namlowetsa m'nyumba mwace. Ndipo iye anamfotokozera Labani zinthu zonsezo.
14 Ndipo Labani anati kwa iye, Etu, iwe ndiwe pfupa langa ndi thupi langa. Ndipo anakhala naye nthawi ya mwezi umodzi.
15 Ndipo Labani anati kwa Yakobo, Cifukwa iwe ndiwe mbale wanga, kodi udzanditumikira ine kwacabe? Undiuze ine, malipiro ako adzakhala otani?
16 Ndipo Labani anali ndi ana akazi awiri, dzina la wamkuru ndi Leya, dzina la wamng'ono ndi Rakele.
17 Maso a Leya anali ofok a, koma Rakele anali wokoma thupi ndi wokongola.
18 Ndipo Yakobo anamkonda Rakele, nati, Ndidzakutumikirani inu zaka zisanu ndi ziwiri cifukwa ca Rakele mwana wanu wamkazi wamng'ono.
19 Ndipo anati Labani, Kuli kwabwino kuti ndimpatse iwe osampatsa kwa mwamuna wina; ukhalebe ndi ine.
20 Ndipo Yakobo anamtumikira zaka zisanu ndi ziwiri cifukwa ca Rakele; koma zidamuonekera iye ngati masiku owerengeka cifukwa ca cikondi cimene anamkonda iye naco.
21 Ndipo Yakobo anati kwa Labani, Undipatse Ine mkazi wanga, cifukwa masiku anga atha, kuti ndilowe kwa iye.
22 Ndipo Labani anasonkhanitsa anthu onse a kumeneko nakonzera madyerero.
23 Ndipo panali madzulo Labani anatenga Leya mwana wace wamkazi, nadza naye kwa Yakobo, ndipo iye analowa kwa mkaziyo.
24 Ndipo Labani anampatsa mwana wace wamkazi Leya Zilipa mdzakazi wace kuti akhale mdzakazi wa Leya.
25 Ndipo panali m'mamawa, anaona kuti ndi Leya; ndipo anati kwa Labani, Ciani wandicitira ine? Kodi sindinakutumikira iwe cifukwa ca Rakele? wandinyenga ine bwanji?
26 Ndipo Labani anati, Satero kwathu kuno, kupatsa wamng'ono asanapatse wamkuru.
27 Umarize sabata lace la uyu, ndipo ndidzakupatsa uyonso cifukwa ca utumiki umene udzanditumikirawo kuonjezera zaka zina zisanu ndi ziwiri.
28 Yakobo ndipo anacita cotero namariza sabata lace; ndipo Labani anampatsa iye Rakele mwana wace wamkazi kuti akwatire iyenso.
29 Ndipo Labani anampatsa mwana wace wamkazi Rakele Biliha mdzakazi wace kuti akhale mdzakazi wa Rakele.
30 Ndipo Yakobo analowanso kwa Rakele, namkondanso Rakele kopambana Leya, namtumikira Labani zaka zisanu ndi ziwiri zinanso.
31 Pamene Yehova anaona kuti anamuda Leva, anatsegula m'mimba mwace; koma Rakele anali wouma.
32 Ndipo Leyaanatenga pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Rubeni; pakuti anati, Cifukwa kuti tsopano mwamuna wanga adzandikonda ine.
33 Ndipo anatenganso pakati, nabala mwana wamwamuna nati, Cifukwa anamva Yehova kuti anandida ine, anandipatsa ine mwana wamwamuna uyunso; ndipo anamucha dzina lace Simeoni.
34 Ndipo anatenganso pakati nabala mwana wamwamuna, nati, Tsopano lino mwamuna wanga adzadziphatika kwa ine cifukwa ndambalira iye ana amuna atatu; cifukwa cace anamucha dzina lace Levi.
35 Ndipo anatenganso pakati nabala mwana wamwamuna; nati, Tsopano ndidzamyamikira Yehova; cifukwa cace anamucha dzina lace Yuda; pamenepo analeka kubala.
1 Pamene Rakele anaona kuti sanambalira Yakobo ana, Rakele anamcitira mkuru wace nsanje; nati kwa Yakobo, Ndipatse ana ndingafe.
2 Ndipo Yakobo anapsa mtima ndi Rakele; nati, Kodi ine ndikhala m'malo a Mulungu amene akukaniza iwe zipatso za mimba?
3 Ndipo Rakele anati, Taonani mdzakazi wanga Biliha, mulowe kwa iye; ndipo iye adzabala pa maondo anga, kuti inenso ndionerepo ana pa iye.
4 Ndipo Rakele anampatsa iye Biliha mdzakazi wace akhale mkazi wace; ndipo Yakobo analowa kwa iye.
5 Ndipo Biliha anatenga pakati, nambalira Yakobo mwana wamwamuna.
6 Rakele ndipo anati, Mulungu wandiweruzira ine, namva mau anga, nandipatsa ine mwana; cifukwa cace anamucha dzina lace Dani.
7 Ndipo Biliha mdzakazi wace wa Rakele anatenganso pakati, nambalira Yakobo mwana wamwamuna waciwiri.
8 Ndipo Rakele anati, Ndi malimbano a Mulungu ndalimbana naye mkuru wanga, ndipo ndapambana naye; ndipo anamucha dzina lace Nafitali.
9 Pamene Leya anaona kuti analeka kubala, anatenga Zilipa mdzakazi wace, nampatsa iye kwa Yakobo kuti akhale mkazi wace.
10 Ndipo Zilipa mdzakazi wace wa Leya anambalira Yakobo mwana wamwamuna.
11 Ndipo Leyaanati, Wamwai ine! ndipo anamucha dzina lace Gadi.
12 Ndipo Zilipa mdzakazi wa Leya anambalira Yakobo mwana wamwamuna waciwiri.
13 Ndipo Leya anati, Ndakondwa inel cifukwa kuti ana akazi adzandicha ine wokondwa: ndipo anamucha dzina lace Aseri.
14 Ndipo Rubeni ananka masiku akudula tirigu, napeza zipatso za mankhwala a cikondi m'thengo, nazitengera kwa amace Leva, Ndipo Rakele anati kwa Leya, Undipatseko mankhwala a mwana wako.
15 Ndipo iye anati kwa Rakele, Kodi mpacabe kuti iwe wacotsa mwamuna wanga? Kodi ufuna kucotsanso mankhwala a mwana wanga? Rakele ndipo anati, Cifukwa cace iye adaagona nawe usiku uno cifukwa ca mankhwala a mwana wako.
16 Ndipo Yakobo anadza madzulo kucokera kumunda, ndipo Leya ananka kukomana naye, nati, Ulowe kwa ine cifukwa ndakulipilira iwe ndi mankhwala a mwana wanga. Ndipo anagona naye usiku womwewo.
17 Ndipo Mulungu anamvera Leya, ndipo anatenga pakati, nambalira Yakobo mwana wamwamuna wacisanu.
18 Ndipo Leya anati, Mulungu wandipatsa ine mphotho yanga, cifukwa ndapatsa mdzakazi wanga kwa mwamuna wanga: namucha dzina lace lsakara.
19 Ndipo Leya anatenganso pakati nambalira Yakobo mwana wamwamuna wacisanu ndi cimodzi.
20 Ndipo Leya anati, Mulungu anandipatsa ine mphatso yabwino; tsopane mwamuna wanga adzakhala ndi ine, cifukwa ndambalira iye ana amuna asanu ndi mmodzi; ndipo anamucha dzina lace Zebuloni.
21 Pambuyo pace ndipo anabala mwana wamkazi, namucha dzina lace Dina.
22 Ndipo Mulungu anakumbukila Rakele, ndipo Mulungu anamvera iye, natsegula m'mimba mwace.
23 Ndipo anatenga pakati, nabala mwana wamwamuna, nati, Mulungu wacotsa manyazi anga;
24 namucha dzina lace Yosefe; ndipo anati, Yehova anandionjezera ine mwana wamwamuna wina.
25 Ndipo panali pamene Rakele anabala Yosefe, Yakobo anati kwa Labani, Undisudzule ine ndinke kwathu ku dziko langa.
26 Undipatse ine akazi anga ndi ana anga cifukwa ca iwowa ndakutumikira iwe, ndimuke: cifukwa udziwa iwe nchito imene ndinakugwirira iwe.
27 Ndipo Labani anati kwa iye, Ngatitu ndikapeza ufulu pamaso pako, ukhale, cifukwa ndazindikira kuti Yehova wandidalitsa ine cifukwa ca iwe.
28 Ndipo iye anati, Undipangire ine malipiro ako, ndipo ndidzakupatsa.
29 Ndipo iye anati kwa Labani, Udziwa iwe comwe ndakutumikira iwe ndi comwe zacita zoweta zako ndi ine.
30 Cifukwa ndisadafike ine, iwe unali nazo zowerengeka, ndipo zacuruka zambirimbiri; Yehova wakudalitsa iwe kuli konse ndinayendako: tsopano ndidzamanga liti banja langa?
31 Ndipo iye anati, Ndikupatsa iwe bwanji? Ndipo Yakobo anati, Usandipatse ine kanthu; ukandicitira ine cotero, ine ndidzadyetsanso ndi kusunganso ziweto zako.
32 Ndidzapita ine lero pakati pa ziweto zonse ndi kusankhasankha m'menemo zoweta zonse zamathotho-mathotho ndi zamaanga-maanga, ndi za nkhosa zonse, ndi mbuzi zonse zamaangamaanga ndi zamathotho-mathotho: zotero zidzakhala malipiro anga.
33 Cotero cilungamo canga cidzandibvomereza m'tsogolomo, pamene udzandifika cifukwa ca malipiro amene ali patsogolo pako; iri yonse yosakhala yamathotho-mathotho ndi yamaanga-maanga ya mbuzi, ndi iri yonse ya mbuzi yosakhala yakuda, ikapezedwa ndi ine, udzaiyesa yakuba.
34 Ndipo Labani anati, Taona, kukhale monga mau ako.
35 Tsiku lomwelo Labani anacotsa atonde amene anali amipyololo-mipyololo ndi amathotho-mathotho, ndi mbuzi zazikazi zinali zamaanga-maanga ndi zamathotho-mathotho zonse zinali zoyera pang'ono, ndi zakuda zonse za nkhosa, napatsa m'dzanja la ana ace amuna.
36 Ndipo iye yekha anatalikitsana ndi Yakobo ulendo wa masiku atatu: ndipo Yakobo anadyetsa ziweto zina za Labani.
37 Ndipo Yakobo anatenga nthyole za mtengo wowisi walibne, ndi za mtengo wakatungurume, ndi za mtengo waarimoni, nakupula m'menemo mizere yoyera, naonetsa moyera mwa m'nthyolemo.
38 Ndipo anaimitsa nthyole zimene anazikupula pandunji ndi zoweta m'micera yakumwera, m'mene ziweto zinafika kumweramo, ndipo zidatenga mabere pamene zinadza kumwa.
39 Ndipo ziweto zinatenga mabere patsogolo pa nthyolezo, ndipo zoweta zinabala zamipyololomipyololo, ndi mathotho-mathotho, ndi zamaanga-maanga.
40 Ndipo Yakobo analekanitsa ana a nkhosa naziika nkhope za zoweta kuti ziyang'anire zamipyololo-mipyololo, ndi zakuda zonse za m'zoweta za Labani, ndipo anaika magulu ace pa okha; sanaziika pa zoweta za Labani.
41 Ndipo panali pamene zoweta zolimba zidatenga mabere, Yakobo anaika nthyole pamaso pa zoweta m'miceramo kuti zitenge mabere pa nthyolezo.
42 Koma pamene ziweto zinali zofoka, sanaziika zimenezo: ndipo zofoka zinali za Labani, ndi zolimba zinali za Yakobo.
43 Munthuyo ndipo anakula kwambiri, nali nazo zoweta zambiri, ndi akapolo amuna ndi akazi, ndi ngamila, ndi aburu.
1 Yakobo afuna kwao nathawa nazo zace, Ndipo anamva mau a ana ace a Labani kuti, Yakobo watenga zonse za atate wathu; m'zinthu zinali za atate wathu wapeza iye cuma ici conse.
2 Ndipo Yakobo anaona nkhope ya Labani, taonani, siinamuonekera iye monga kale.
3 Ndipo Yehova anati kwa Yakobo, Bwera ku dziko la atate wako, ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakhala ndi iwe.
4 Ndipo Yakobo anatumiza naitana Rakele ndi Leya adze kubusa ku zoweta zace,
5 ndipo anati kwa iwo, Ndiona ine nkhope ya atate wanu kuti siindionekera ine monga kale; koma Mulungu wa atate wanga anali ndi ine.
6 Ndipo inu mudziwa kuti ndi mphamvu zanga zonse ndatumikira atate wanu.
7 Ndipo atate wanu wandinyenga ine, nasinthanitsa malipilo anga kakhumi; koma Mulungu sanamlole iye andicitire ine coipa.
8 Akati cotero, Zamathotho-mathotho zidzakhala malipilo ako, zoweta zonse zinabala zamathotho-mathotho; ndipo akati iye cotere, Zamipyololo-mipyololo zidzakhala malipilo ako, ziweto zonse zinabala mipyololo-mipyololo.
9 Comweco Mulungu anazicotsa zoweta za atate wanu, nandipatsa ine.
10 Ndipo panali potenga mabere ziwetozo, ine ndinatukula maso anga, ndipo ndinapenya m'kulota, taonani, atonde okwera ziweto anali amipyololo-mipyololo, amathotho-mathotho, ndi amaanga-maanga.
11 Mthenga wa Mulungu ndipo anati kwa ine m'kulotamo, Yakobo; nati ine, Ndine pano,
12 Ndipo anati, Tukulatu maso ako, nuone, atonde onse amene akwera zoweta ali amipyololo-mipyololo, amathotho-mathotho, ndi amaangamaanga: cifukwa ndaona zonse zimene Labani akucitira iwe.
13 Ine ndine Mulungu wa ku Beteli, kuja unathira mafuta pamwala paja, pamene unandilumbirira ine cilumbiriro: tsopano uka, nucoke m'dziko lino, nubwerere ku dziko la abale ako.
14 Ndipo Rakele ndi Leya anayankha, nati kwa iye, Kodi tiri nalonso gawo kapena colowa m'nyumba ya atate wathu?
15 Kodi satiyesa ife alendo? cifukwa anatigulitsa ife, nathanso kuononga ndalama zathu.
16 Cifukwa kuti cuma conse Mulungu anacicotsa kwa atate wathu ndi cathu ndi ca ana athu; tsono, zonse wakunenera iwe Mulungu, ucite.
17 Ndipo anauka Yakobo nakweza ana ace ndi akazi ace pa ngamila;
18 ndipo ananka nazo zoweta zace zonse, ndi cuma cace conse anacisonkhanitsa, zoweta zace anaziona m'Padan-aramu, kuti anke kwa Isake atate wace ku dziko la Kanani.
19 Ndipo Labani ananka kukasenga nkhosa zace: ndipo Rakele anaba aterafi a atate wace.
20 Ndipo Yakobo anathawa kwa Labani Msuriyamobisika, m'mene sanamuuzeiye kuti analinkuthawa.
21 Ndipo anathawa iye ndi zonse anali nazo: ndipo anauka naoloka panyanja naloza nkhope yace iyaog'anire ku phiri la Gileadi.
22 Tsiku lacitatu anamuuza Labani kuti Yakobo wathawa.
23 Ndipo iye anatenga abale ace pamodzi naye, namlondola iye ulendo wa masiku asanu ndi awiri: nampeza iye pa phiri la Gileadi.
24 Ndipo Mulungu anadza kwa Labani Msuriya usiku, nati kwa iye, Tadziyang'anira wekha, usanene kwa Yakobo kapena zabwino kapena zoipa,
25 Ndipo Labani anakomana naye Yakobo. Ndipo Yakobo anamanga hema wace m'phirimo: ndipo Labani ndi abale ace anamanga m'phiri la Gileadi.
26 Ndipo Labani anati kwa Yakobo, Wacitanji? Wathawa kwa ine mobisika ndi kutenga ana anga akazi, monga mikoli ya lupanga.
27 Wathawanji iwe mobisika, ndi kundicokera kutseri, osandiuza ine, kuti ndikadakumukitsa iwe ndi kusekerera ndi nyimbo ndi lingaka ndi zeze?
28 Ndipo sunandiloleza ine ndimpsompsone ana anga amuna ndi akazi? wapusa iwe pakucita cotero.
29 M'dzanja langa muli mphamvu yakucitira iwe zoipa koma Mulungu wa atate wako anati kwa ine usiku walero, kuti, Tadziyang'anira wekha, usanene kwa Yakobo kapena zabwino kapena zoipa.
30 Tsono ungakhale ukadamuka cifukwa mtima wako ulinkukhumba nyumba ya atate wako, bwanji waba iwe milungu yanga?
31 Ndipo anayankha Yakobo nati kwa Labani, Cifukwa ndinaopa: cifukwa kuti, ndinati, Kapena udzandilanda ine ana ako akazi.
32 Ali yense umpeza ali nayo milungu yako, asakhale ndi movo: pamaso pa abale athu, tayang'anira zako ziri ndi ine, nuzitenge wekha. Pakuti sanadziwe Yakobo kuti Rakele anaiba.
33 Ndipo Labani analowa m'hema wa Yakobo, ndi m'hema wa Leya, ndi m'mahema a adzakazi awiri aja; koma sanapeze, Ndipo anaturuka m'hema wa Leya nalowa m'hema wa Rakele.
34 Ndipo Rakele anatenga aterafiwo nabisa pa cokhalira ca ngamila, nakhala pamenepo, Ndipo Labani anafunafuna m'hema monse, koma sanawapeze.
35 Ndipo Rakele anati kwa atate wace, Asakwiye mbuyanga kuti sindingathe kuuka pamaso panu; cifukwa zocitika pa akazi ziri pa ine. Ndipo Labani anafunafuna koma sanapeze aterafiwo.
36 Ndipo anakwiya Yakobo namkalipira Labani: ndipo Yakobo anayankha nati kwa Labani, Kodi ndacimwa ciani? ucimo wanga nguti, kuti unanditsatatsata ine pambuyo panga?
37 Pakuti wafunafuna monse ndiri nazo, kodi wapeza ciani pa zinthu za m'nyumba mwako? Tafika naco apa pa abale anga ndi ako, kuti aweruze pa ife tonse awiri.
38 Zaka makumi awiriwo ndakhala nawe, nkhosa ndi mbuzi zako zazikazi sizinapoloze, ndi abira a zoweta zako sindinadye.
39 Cimene cinazomoledwa ndi cirombo sindinacitengere kwa iwe; ndekha ndinalipira; pa dzanja langa unacifuna, cingakhale cobedwa kapena pausiku kapena pausana.
40 Cotero ndinakhala; usana ludzu linakomola ine, usiku cisanu; tulo tanga tinacoka m'maso mwanga.
41 Ndinakhala cotere zaka makumi awiri m'nyumba mwako; zaka khumi ndi zinai ndinakutumikira iwe cifukwa ca ana ako akazi awiri, ndi zaka zisanu ndi cimodzi cifukwa ca zoweta zako; wasintha malipiro anga kakhumi.
42 Mulungu wa atate wanga, Mulungu wa Abrahamu, ndi Kuopsa kwa Isake zikadapanda kukhala ndi ine, ukadandicotsa ine wopanda kanthu m'manja. Mulungu anakuona kusauka kwanga, ndi nchito ya manja anga, ndipo anadzudzula iwe usiku walero.
43 Ndipo Labani anayankha nati kwa Yakobo, Akaziwa ndiwo ana anga, anawa ndiwo ana anga, zowetazi ndizo zoweta zanga ndi zonse ulinkuziona ndizo zanga: nanga ndidzacitira ine ciani lero kwa ana anga akazi amenewa, kapena ana ao amene anabala?
44 Tsopano tiyeni tipangane pangano, ine ndi iwe; likhale mboni pakati pa ine ndi iwe.
45 Ndipo Yakobo anatenga mwala, nauimiritsa.
46 Ndipo Yakobo anati kwa abale ace, Sonkhanitsani miyala; ndipo anasonkhanitsa miyala nakundika mulu: ndipo anadya pamulupo.
47 Ndipo Labani anacha pamenepo Yegara-sahaduta; koma Yakobo anacha Galeeda.
48 Ndipo Labani anati, Muluwu ndiwo mboni pakati pa ine ndi iwe lero. Cifukwa cace anacha dzina lace, Galeeda;
49 ndi Mizipa, cifukwa kuti anati, Yehova ayang'anire pakati pa ine ndi iwe, pamene tisiyana wina ndi mnzace.
50 Ukasautsa ana anga akazi, kapena ukatenga akazi kuonjezera pa ana anga, palibe munthu mmodzi ali nafe; taonani, Mulungu ndiye mboni yanga ndi yako.
51 Ndipo Labani anati kwa Yakobo. Taona muluwu, taona coimiritsaci, ndaciimiritsa pakati pathu.
52 Muluwu ndiwo mboni, coimiritsaci ndico mboni, kuti ine sindidzapitirira pa muluwu kunka kwa iwe, ndipo iwe sudzapitirira pa muluwu ndi pa coimiritsaci kudza kwa ine kuti ticitirane zoipa,
53 Mulungu wa Abrahamu ndi Mulungu wa Nahori, Mulungu wa atate wao aweruze pa ife. Ndipo Yakobo analumbirira pa Kuopsa kwa atate wace Isake.
54 Ndipo Yakobo anapereka nsembe paphiripo, naitana abale ace kuti adye cakudya; ndipo anadya cakudya, nagona paphiripo usiku wonse.
55 M'mamawa Labani anauka nampsompsona ana ace amuna ndi akazi, nawadalitsa: ndipo Labani anacoka, nabwera kumalo kwace.
1 Ndipo Yakobo anankabe ulendo wace, ndipo amithenga a Mulungu anakomana naye.
2 Pamene Yakobo anawaona anati, Ili ndi khamu la Mulungu: ndipo anacha pamenepo dzina lace Mahanaimu.
3 Ndipo Yakobo anatumiza amithenga patsogolo pace kwa Esau mkuru wace, ku dziko la Seiri, ku dera la ku Edomu.
4 Ndipo anauza iwo kuti, Mukanene cotere kwa mbuyanga Esau: Atero Yakobo kapolo wako, ndakhala pamodzi naye Labani, ndipo ndakhalabe kufikira tsopano line:
5 ndipo ndiri nazo ng'ombe ndi aburu, ndi zoweta ndi akapolo ndi adzakazi, ndipo ndatumiza kukuuza mbuyanga kuti ndipeze ufulu pamaso pako.
6 Ndipo amithenga anabwera kwa Yakobo kuti, Tidafika kwa mbale wanu Esau, ndipo iyenso alinkudza kukomana nanu, ndipo ali nao anthu mazana anai.
7 Ndipo Yakobo anaopa kwambiri, nabvutidwa; ndipo anagawa anthu anali nao ndi nkhosa ndi zoweta, ndi ngamila, zikhale makamu awiri;
8 ndipo anati, Akafika Esau pa khamu limodzi nalikantha, linalo lotsala lidzapulumuka.
9 Ndipo Yakobo anati, Mulungu wa atate wanga Abrahamu, Mulungu wa atate wanga Isake, Yehova, amene munati kwa ine, Bwera ku dziko lako, ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakucitira iwe bwino:
10 sindiyenera zazing'ono za zifundo zonse, ndi zoona zonse, zimene mwamcitira kapolo wanu: cifukwa ndi ndodo yanga ndinaoloka pa Yordano uyu; ndipo tsopano ndiri makamu awiri.
11 Mundipulumutsetu ine m'dzanja la mkuru wanga, m'dzanja la Esau; cifukwa ine ndimuopa iye, kapena adzadza kudzandikantha ine, ndi amai pamodzi ndi ana.
12 Ndipo Inu munati. Ndidzakucitira iwe bwino ndithu, ndidzakuyesa mbeu yako monga mcenga wa pa nyanja yaikuru, umene sungathe kuwerengeka cifukwa ca unyinji wace.
13 Ndipo anagona komweko usiku womwewo, natengako zimene anali nazo, mphatso yakupatsa Esau mkuru wace:
14 mbuzi zazikazi mazana awiri, atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi mazana awiri, ndi zazimuna makumi awiri,
15 ngamila zamkaka makumi atatu ndi ana ao, ng'ombe zazikazi makumi anai, zazimuna khumi, aburu akazi makumi awiri ndi ana khumi.
16 Ndipo anazipereka zimenezo m'manja a anyamata ace, gulu pa lokha gulu pa lokha: ndipo anati kwa anyamata ace, Taolokani patsogolo panga, tacitani danga pakati pa magulu, tina ndi lina.
17 Ndipo anauza wotsogolera kuti, Pamene akomana nawe mkuru wanga Esau ndi kufunsa iwe kuti, Ndiwe yani, umuka kuti? za yani zimenezi patsogolo pako?
18 pomwepo uziti, Za kapolo wanu Yakobo; ndizo mphatso yotumizidwa kwa mbuyanga Esau; taonani ali pambuyo pathu.
19 Ndipo anauzanso waciwiri ndi wacitatu, ndi onse anatsata magulu, kuti, Muzinena kwa Esau cotero, pamene mukomana naye:
20 ndiponso muziti, Ndiponso, taonani, kapolo wanu Yakobo ali pambuyo pathu, Pakuti anati, Ndidzampembedzera iye ndi mphatso imene ipita patsogolo panga, pambuyo pace ndidzaona nkhope yace; kapena adzandilandira ine.
21 Momwemo naolotsa mphatso patsogolo pace: ndipo iye yekha anagona usiku womwewo pacigono.
22 Ndipo anauka usiku womwewo, natenga akazi ace awiri, ndi adzakazi ace awiri, ndi ana ace amuna khumi ndi mmodzi, naoloka pa doko la Yaboki.
23 Ndipo anawatenga iwo nawaolotsa pamtsinje, naziolotsa zonseanalinazo.
24 Ndipo anatsala Yakobo yekha; ndipo analimbana naye munthu kufikira mbandakuca.
25 Ndipo pamene anaona kuti sanamlaka, anakhudza nsukunyu ya ncafu yace; ndipo nsukunyu ya ncafu yace ya Yakobo inaguluka, pakulimbana naye.
26 Ndipo iye anati Ndileke ndimuke, cifukwa kulinkuca. Ndipo Yakobo anati, Sindidzakuleka iwe kuti umuke, ukapanda kundidalitsa ine.
27 Ndipo iye anati kwa Yakobo, Dzina lako ndani? Nati iye, Yakobo.
28 Ndipo anati, Dzina lako silidzachedwanso Yakobo, koma Israyeli, cifukwa unayesana naye Mulungu ndithu, ndipo unapambana.
29 Yakobo ndipo anafunsa iye, nati, Undiuze ine dzina lako. Ndipo iye anati, Undifunsa dzina cifukwa ninji? Ndipo anamdalitsa iye pamenepo.
30 Ndipo anacha dzina la malo amenewo, Penieli: cifukwa ndaonana ndi Mulungu nkhope ndi nkhope, ndipo wapulumuka moyo wanga,
31 Ndipo kudamcera iye pamene analoloka pa Penieli, ndipo iye anatsimphina ndi ncafu yace.
32 Cifukwa cace ana a Israyeli samadya ntsempha ya thako iri pa nsukunyu ya ncafu kufikira lero: cifukwa anakhudza nsukunyu ya ncafu ya Yakobo pa ntsempha ya thako.
1 Ndipo Yakobo anatukula maso ace, taonani, anadza Esau, ndi pamodzi naye anthu mazana anai. Ndipo anagawira ana kwa Leya, ndi kwa Rakele, ndi kwa adzakazi awiri aja.
2 Ndipo anaika adzakazi ndi ana ao patsogolo, ndi Leya ndi ana ace pambuyo pao, ndi Rakele ndi Yosefe pambuyo pa onse.
3 Ndipo iye mwini anatsogolera patsogolo pao, nawerama pansi kasanu ndi kawiri mpaka anayandikira mkuru wace.
4 Ndipo Esau anathamangira kukomana naye namfungatira, nagwa pankhope pace, nampsompsona; ndipo analira iwo.
5 Ndipo anatukula maso ace nawaona akazi ndi ana; nati, Ndani awa ali ndi iwe? Ndipo iye anati, Ndiwo ana amene Mulungu anakomera mtima kumpatsa kapolo wanu.
6 Ndipo adzakazi anayandikira ndi ana ao, nawerama pansi.
7 Ndiponso Leya ndi ana ace anayandikira nawerama pansi: pambuyo pace anayandikira Yosefe ndi Rakele, nawerama pansi,
8 Ndipo anati, Nanga khamu lonse limene ndinakomana nalo nlotani? Ndipo anati, Kuti ndipeze ufulu pamaso pa mbuyanga.
9 Ndipo Esau anati, Zanga zindifikira; mbale wanga, khala nazo zako iwe wekha.
10 Ndipo! Yakobo anati, Iaitu, ngatitu ndapeza ufulu pamaso panu, mulandire mphatso yanga pa dzanja langa; pakuti popeza ndinaona nkhope yanu, monga anthu aona nkhope ya Mulungu, ndipo inu mwanelibvomereza ine.
11 Landiranitu mdalitso wanga umene wafika kwa inu, pakuti Mulungu wandicitira ine zaufulu, ndipo zanganso zindifikira. Ndipo anamkakamiza, nalandira.
12 Ndipo Esau anati, Tiyeni timuke; nditsogolera ndine.
13 Ndipo anati kwa iye, Mbuyanga adziwa kuti ana ali ambowa, ndipo nkhosa ndi zoweta ndiri nazo zirinkuyamwitsa: ndipo akathamangitsa tsiku limodzi zoweta zonse zidzafa.
14 Mbuyanga atsogoleretu kapolo wace, ndipo ine ndidzazitsogolera pango'no-pang'ono monga mwa mayendedwe a zoweta ziri pamaso panga, ndi monga mwa mayendedwe a ana, mpaka ndifike kwa mbuyanga ku Seiri.
15 Ndipo Esau anati, Ndikusiyire anthu ena amene ali ndi ine, Ndipo iye anati, Cifukwa canji? ndipeze ine ufulu pamaso pa mbuyanga.
16 Ndipo Esau anabwera tsiku lomwelo kunka ku Seiri.
17 Ndipo Yakobo anankabe ulendo wace ku Sukoti, namanga nyumba yace pamenepo, namanga makola a zoweta zace: cifukwa cace dzina lace la kumeneko ndi Sukoti.
18 Ndipo Yakobo anafika ndi mtendere ku mudzi wa Sekemu umene uli m'dziko la Kanani, pamene anacokera ku Padanaramu; namanga tsasa pandunji pa mudzipo.
19 Ndipo anagula ndi ndalama zana limodzi dera la munda kumeneko anamanga bema wace, pa dzanja la ana ace a Hamori atate wace wa Sekemu.
20 Ndipo anamanga pamenepo guwa la nsembe, nacha pamenepo EleloheIsrayeli.
1 Ndipo Dina mwana wamkazi wa Leya, amene anambalira Yakobo, ananka kukaona akazi a kumeneko.
2 Pamene anamuona iye Sekemu, mwana wace wamwamuna wa Hamori Mhivi, karonga wa dzikolo, anamtenga nagona ndi iye, namuipitsa,
3 Ndipo mtima wace unakhumba Dina mwana wace wamkazi wa Yakobo, ndipo anamkonda namwaliyo, nanena momkopa namwaliyo.
4 Ndipo anati Sekemu kwa atate wace Hamori kuti, Munditengere ine mkazi uyo akhale mkazi wanga.
5 Ndipo anamva Yakobo kuti anamuipitsa Dina, mwana wace wamkazi; ana ace amuna anali ndi zoweta zace kudambo: ndipo Yakobo anakhala cete mpaka anafika iwo.
6 Ndipo Hamori atate wace wa Sekemu anaturuka kunka kwa Yakobo kukanena ndi iye.
7 Ndipo pakumva ico ana ace amuna a Yakobo anabwera pocokera kudambo: amunawo ndipo anaphwetekwa mtima, nakwiya kwambiri, cifukwa iyeyo anacita copusa coipira Israyeli pakugona ndi mwana wamkazi wa Yakobo; ndico cosayenera kucita.
8 Ndipo Hamori ananena ndi iwo, kuti, Mtima wa Sekemu mwana wanga umkhumba mwana wako wamkazi: umpatsetu kuti akhale mkazi wace.
9 Mukwatirane ndi ife: tipatseni ife ana anu akazi, ndiponso dzitengereni ana athu akazi.
10 Ndipo mudzakhala pamodzi ndi ife, dziko lidzakhala pamaso panu; khalani m'menemo ndi kucita malonda, ndi kukhala nazo zanuzanu m'menemo.
11 Ndipo Sekemu anati kwa atate wace wa mkazi ndi kwa abale ace, Tipeze ufulu pamaso panu, cimene mudzanena kwa ine ndidzapereka.
12 Mundipemphe ine za mitulo ndi zaulere zambirimbiri, ndipo ndidzapereka monga mudzanena kwa ine; koma mundipatse ine namwaliyo akhale mkazi wanga.
13 Ndipo ana ace amuna a Yakobo anayankha Sekemu ndi Hamori atate wace monyenga, nanena, popeza anamuipitsa Dina mlongo wao,
14 nati kwa iwo, Sitingathe kucita ici, kupereka mlongo wathu kwa mwamuna wosadulidwa; cifukwa kumeneko ndiko kuticepetsa ife.
15 Koma apa pokha tidzakubvomerezani: ngati mudzakhala onga ife ndi kudulidwa amuna onse;
16 pamenepo tidzakupatsani inu ana athu akazi, ndipo tidzadzitengera ana anu akazi, ndipo tidzakhala pamodzi ndi inu, ndi kukhala mtundu umodzi.
17 Koma mukapanda kutimvera ndi kusadulidwa, pamenepo tidzatenga mwana wathu wamkazi, ndi kumuka naye.
18 Mau ao ndipo anakomera Hamori ndi Sekemu mwana wace wa Hamori.
19 Ndipo mnyamatayo sanacedwa kucicita popeza anakondwera ndi mwana wace wamkazi wa Yakobo; ndipo iye anali wolemekezedwa woposa onse a pa banja la atate wace.
20 Ndipo Hamori ndi Sekemu mwana wace anafika ku cipata ca mudzi wao, nalankhulana ndi anthu a mudzi wao, kuti,
21 Anthu amenewa ali amtendere pamodzi ndi ife; cifukwa cace akhale m'dzikomo, acite malonda m'menemo: pakuti taonani dzikololirilalikurulokwaniraiwo; tidzitengere ana ao akazi akhale akazi athu, tiwapatse amenewa ana athu akazi.
22 Anthuwo adzatiloleza ife tikhale nao anthu amodzi, pokhapo amuna onse a mwa ife adzadulidwa, monga iwo adulidwa.
23 Kodi ng'ombe zao ndi cuma cao ndi zoweta zao sizidzakhala zathu? Pokhapo tibvomerezana nao ndipo adzakhala pamodzi ndi ife.
24 Ndipo onse amene anaturuka pa cipata ca mudzi wao anamvera Hamori ndi mwana wace Sekemu, nadulidwa amuna onse akuturuka pa cipata ca mudzi wao.
25 Ndipo panali tsiku lacitatu pamene anamva kuwawa, ana amuna awiri a Yakobo, Simeoni ndi Levi, abale ace a Dina, anatenga wina lupanga lace wina lace, nalimbika mtima nalowa m'mudzi napha amuna onse.
26 Ndipo anapha Hamori ndi Sekemu mwana wace ndi lupanga, naturutsa Dina m'nyumba ya Sekemu nacoka naye.
27 Ndipo ana amuna a Yakobo anadzakwa ophedwa nafunkhamudzi cifukwa anamuipitsa mlongo wao.
28 Ndipo analanda nkhosa zao ndi zoweta zao ndi aburu ao, ndi za m'mudzi, ndi za m'munda;
29 ndi cuma cao conse ndi ana ao ndi akazi ao anawagwira, nafunkha zonse za m'nyumba.
30 Ndipo Yakobo anati kwa Simeoni ndi Levi, Mwaodisautsa ndi kundinunkhitsa ine mwa anthu okhala m'dzikomu, mwa Akanani ndi mwa Aperezi; ndipo ine ndine wa anthu owerengeka, adzandisonkhanira ine ndi kundikantha: ndipo ndidzapasulidwa ine ndi a pa nyumba yanga.
31 Ndipo iwo anati, Kodi iye ayenera kusandutsamloogo wathu wadama?
1 Ndipo Mulungu anati kwa Yakobo, Nyamuka nukwere kunka ku Beteli nukhale kumeneko: numange kumeneko guwa la nsembe la Mulungu amene anaonekera kwa iwe pamene unathawa ku nkhope ya Esau mbale wako.
2 Ndipo Yakobo anati kwa a banja lace, ndi kwa onse amene anali ndi iye, Cotsani milungu yacilendo iri mwa inu, mudziyeretse, ndi kupindula zobvala zanu:
3 tinyamuke, tikwere tinke ku Beteli: ndipo tidzamanga kumeneko guwa la nsembe la Mulungu amene anandibvomereza tsiku la mabvuto anga, ndiponso anali ndi ine m'njira m'mene ndinapitamo.
4 Ndipo anampatsa Yakobo milungu yacilendo yonse inali m'manja mwao, ndi mphete zinali m'makutu mwao: ndipo Yakobo anazibisa pansi pa mtengo wathundu unali pa Sekemu.
5 Ndipo anapita, ndipo kuopsa kwa Mulungu kudagwera midzi yakuwazinga, ndipo sanalondola ana a Yakobo.
6 Ndipo Yakobo anafika ku Luzi, ndiko ku dziko la Kanani (ndiwo Beteli), iye ndi anthu onse anali pamodzi ndi iye.
7 Ndipo anamanga kumeneko guwa la nsembe, Dacha pamenepo El Beteli: pakuti kumeneko Mulungu anaonekera kwa iye muja anathawa pa nkhope ya mbale wace.
8 Ndipo anafa Debora mlezi wa Rebeka, naikidwa kunsi kwa Beteli, pansi pa mtengo wathundu; ndipo anacha dzina lace AlioniBakuti.
9 Ndipo Mulungu anamuonekeranso Yakobo, pamene iye anacokera m'Padanaramu, namdalitsa iye.
10 Ndipo Mulungu anati kwa iye, Dzina lako ndi Yakobo; dzina lako silidzachedwanso Yakobo, koma dzina lako lidzakhala Israyeli: ndipo anamucha dzina lace Israyeli.
11 Ndipo Mulungu anati kwa iye, Ine ndine Mulungu Wamphamvuyonse: ubale, ucuruke; mwa iwe mudzaturuka mtundu ndi gulu la mitundu, ndipo mafumu adzaturuka m'cuuno mwako;
12 ndipo dziko limene ndinapatsa kwa Abrahamu ndi kwa Isake ndidzalipatsa kwa iwe ndipo ndidzapatsa mbeu zako za pambuyo pako dzikoli.
13 Ndipo Mulungu anakwera kumcokera iye kumene ananena naye.
14 Ndipo Yakoboanaimiritsamwala pamalo pamene ananena ndi iye, coimiritsa camwala: ndipo anathira pamenepo nsembe yothira, nathirapo mafuta.
15 Ndipo anacha dzina lace la pamalo pamene Mulungu ananena ndi iye, Beteli.
16 Ndipo anacokera ku Beteli: ndipo panatsala nthawi asanafike ku Efrati: ndipo Rakele anabala nabvutidwa.
17 Ndipo panali pamene anabvutidwa, namwino anati kwa iye, Usaope: pakuti udzakhala ndi mwana wina wamwamuna.
18 Ndipo pakutsirizika iye, pakuti anamwalira, anamucha dzina lace Benoni; koma atate wace anamucha Benjamini.
19 Ndipo anafa Rakele, naikidwa pa njira va ku Efrati (ndipo Betelehemu),
20 Ndipo Yakobo anaimiritsa mwala pamanda pace: umenewo ndi coimiritsa ca pa manda a Rakele kufikira lero.
21 Ndipo Israyeli anapita namanga hema wace patseri pa nsanja ya Edere.
22 Ndipo panali pamene Israyeli anakhala m'dzikomo, Rubeni anamuka nagona ndi Biliha, mkazi wamng'ono wa atate wace: ndipo Israyeli anamva. Ana amuna a Yakobo anali khumi ndi awiri:
23 ana amuna a Leya: ndiwo Rubeni mwana woyamba wa Yakobo, ndi Simeoni ndi Levi, ndi Yuda, ndi Zebuloni, ndi Isakara;
24 ana amuna a Rakele: ndiwo Yosefe ndi Benjamini;
25 ana amuna a Biliha mdzakazi wace wa Rakele: ndiwo Dani ndi Nafitali;
26 ndipo ana amuna a Zilipa mdzakazi wace wa Leya: ndiwo Gadi ndi Aseri: amenewo ndi ana amuna a Yakobo amene anabala iye m'Padanaramu.
27 Ndipo Yakobo anafika kwa Isake atate wace ku Mamre, ku KiriyatiAriba (ndiwo Hebroni) kumene anakhala Abrahamu ndi Isake.
28 Ndipo masiku a Isake anali zaka zana limodzi kudza makumi asanu ndi atatu.
29 Ndipo Isake anatsirizika nafa, nasonkhanitsidwa kwa anthu a mtundu wace, wokalamba ndi wa masiku okwanira: ndipo Esau ndi Yakobo ana ace amuna anamuika iye.
1 Mibadwo ya Esau (ndiye Edomu) ndi iyi:
2 Esau anatenga akazi ace a ana akazi a m'Kanani: Ada mwana wamkazi wa Eloni Mhiti, ndi Oholibama mwana wamkazi wa Ana, mwana wamkazi wa Zibeoni Mhivi;
3 ndi Basemati mwana wamkazi wa lsmayeli, mlongo wace wa Nabayoti.
4 Ndipo Ada anambalira Esau Elifazi; ndipo Basemati anabala Reueli;
5 ndipo Oholibama anabala Jeusi, ndi Jalamu, ndi Kora; amenewa ndi ana amuna a Esau, amene anambadwira m'dziko la Kanani.
6 Ndipo Esau anatenga akazi ace, ndi ana ace amuna, ndi ana ace akazi, ndi anthu onse a m'banja mwace, ndi ng'ombe zace, ndi zoweta zace, ndi zonse anali nazo anasonkhanitsa m'dziko la Kanani; ndipo ananka ku dziko losiyana patari ndi Yakobo mphwace.
7 Cifukwa cuma cao cinali cambiri cotero kuti sanakhoza kukhala pamodzi; ndipo dziko lokhalamo iwo silinakhoza kuwakwanira cifukwa ca ng'ombe zao.
8 Ndipo Esau anakhala m'phiri la Seiri; Esau ndiye Edomu.
9 Mibadwo ya Esau atate wao wa Aedomu m'phiri la Seiri ndi iyi:
10 amenewa ndi maina a ana amuna a Esau: Elifazi mwana wamwamuna wa Ada, mkazi wace wa Esau, Reueli mwana wamwamuna wa Basemati mkazi wace wa Esau.
11 Ndipo ana amuna a Elifazi ndiwo Temani, Omari, Zefo ndi Gatamu, ndi Kenazi.
12 Ndipo Timna anali mkazi wace wamng'ono wa Elifazi mwana wamwamuna wa Esau; ndipo anambalira Elifazi Amaleki: amenewa ndi ana amuna a Ada mkazi wace wa Esau.
13 Ndi ana amuna a Reueli: Nahati, ndi Zera, Sama, ndi Miza; amenewa ndi ana a Basemati mkazi wace wa Esau.
14 Ana amuna a Oholibama mwana wamkazi wa Ana, mwana wamkazi wa Zibeoni, mkazi wace wa Esau, ndi awa: ndipo iye anambalira Esau Jeusi, ndi Jalamu, ndi Kora.
15 Amenewa ndi mafumu a ana amuna a Esau: ana amuna a Elifazi woyamba wa Esau: mfumu Temani, mfumu Omari, mfumu Zefo, mfumu Kenazi,
16 mfumu Kora, mfumu Gatamu, mfumu Amaleki: amenewa ndi mafumu a kwa Elifazi m'dziko la Edomu: amenewa ndi ana amuna a Ada.
17 Amenewa ndi ana amuna a Reueli mwana wamwamuna wa Esau: mfumu Nahati, mfumu Zera, mfumu Sama, mfumu Miza; amenewa ndi mafumu obadwa kwa Reueli m'dziko la Edomu: amenewa ndi ana amuna a Basemati mkazi wace wa Esau.
18 Amenewa ndi ana amuna a Oholibama mkazi wace wa Esau; mfumu Jeusi, mfumu Jalamu, mfumu Kora, amenewa ndi mafumu obadwa kwa Oholibama mwana wamkazi wa Ana, mkazi wace wa Esau.
19 Amenewa ndi ana amuna a Esau, amenewa ndi mafumu ao; yemweyo ndi Edomu.
20 Amenewa ndi ana amuna a Seiri Mhori, okhala m'dzikomo: Lotani ndi Sobala, ndi Zibeoni, ndi Ana,
21 ndi Disoni ndi Ezeri ndi Disani; amenewa ndi mafumu obadwa kwa Ahori, ana a Seiri, m'dziko la Edomu.
22 Ndi ana a Lotani anali Hori ndi Hemamu: mlongo wace wa Lotani anali Timna.
23 Ana a Sobali ndi awa: Alivani ndi Manahati ndi Ebali, Sefo ndi Onamu.
24 Ana a Zibeoni ndi amenewa: Aia ndi Ana; ameneyo ndiye Ana uja anapeza akasupe a madzi amoto m'cipululu, pakudyetsa aburu a Zibeoni atate wace.
25 Ana a Ana ndi awa: Disoni ndi Oholibama mwana wamkazi wa Ana.
26 Ana a Disoni ndi awa: Hemadani ndi Esibani ndi Itirani, ndi Kerana.
27 Ana a Ezeri ndi awa: Biliha, ndi Zavani, ndi Akani.
28 Ana a Disoni ndi awa: Uzi ndi Arana.
29 Mafumu obadwa kwa Ahori: mfumu Lotani, mfumu Sobali, mfumu Zibeoni, mfumu Ana,
30 mfumu Disoni, mfumu Ezeri, mfumu Disani; amenewa ndi mafumu obadwa kwa Ahori, monga mwa maufumu ao m'dziko la Seiri.
31 Amenewo ndi mafumu analamulira m'dziko la Edomu, asadalamulire ana a Israyeli mfumu ali yense.
32 Ndipo Bela mwana wamwamuna wa Beori, analamulira m'Edomu, ndipo dzina la mudzi wace ndilo Dinaba.
33 Ndipo Bela anamwalira, ndipo Jobabi mwana wamwamuna wa Zera wa ku Bozara analamulira m'malomwace.
34 Ndipo Jobabi anamwalira, ndipo Husami wa ku dziko la Atemani analamulira m'malo mwaceo
35 Ndipo Husami anamwalira, ndipo Hadadi mwana wamwamuna wa Bedadi, amene anakantha Midyani m'dambo la Moabu, analamulira m'malo mwace: dzina la mudzi wace ndi Avita.
36 Ndipo Hadadi anamwalira, ndipo Samila wa ku Masereka analamulira m'malo mwace.
37 Ndipo Samila anamwalira, ndipo Sauli wa ku Rehoboti pambali pa Nyanja analamulira m'malo mwaceo
38 Ndipo Sauli anamwalira, ndipo Baal-hanani mwana wamwamuna wa Akibori analamulira m'malo mwace.
39 Ndipo Baal-hanani mwana wamwamuna wa Akibori anamwalira, ndipo Hadari analamulira m'malo mwace; dzina la mudzi wace ndi Pau; ndipo dzina la mkazi wace ndi Mehetabeli, mwana wamkazi wa Matiredi, mwana wamkazi wa Me-zahabi.
40 Maina a mafumu obadwa kwa Esau, monga mabanja ao, monga malo ao, monga maina ao ndi awa: mfumu Timna, mfumu Aliva, mfumu Jeteti:
41 mfumu Oholibama, mfumu Ela, mfumu Pinoni;
42 mfumu Kenazi, mfumu Temani, mfumu Mibezari;
43 mfumu Magidieli, mfumu Iramu; amenewa ndi mafumu a Edomu, monga mwa kukhala kwao m'dziko lokhala laolao. Uyo ndiye Esau atate wao wa Aedomu.
1 Ndipo Yakobo anakhala m'dziko limene anakhalamo mlendo atate wace, m'dziko la Kanani.
2 Mibadwo ya Yakobo ndi iyi: Yosefe anali wa zaka khumi ndi zisanu ndi ziwiri analinkudyetsa zoweta pamodzi ndi abale ace; ndipo anali mnyamata pamodzi ndi ana a Biliha, ndi ana amuna a Zilipa, akazi a atate wace; ndipo Yosefe anamfotokozera atate wace mbiri yao yoipa.
3 Koma Israyeli anamkonda Yosefe koposa ana ace onse, pakuti anali mwana wa ukalamba wace; ndipo anamsokera iye malaya amwinjiro.
4 Ndipo abale ace anaona kuti atate wace anamkonda iye koposa abale ace onse: ndipo anamuda iye, ndipo sanathe kulankhula ndi iye mwamtendere.
5 Yosefe ndipo analota loto, nawafotokozera abale ace; ndipo anamuda iye koposa.
6 Ndipo iye anati kwa iwo, Tamvanitu loto limene ndalota:
7 pakuti taonani, ndinalinkumanga mitolo m'munda, ndipo taonani, mtolo wanga unauka nuima ciriri! ndipo taonani, mitolo yanu inadza niuzinga kwete, niuweramira mtolo wanga.
8 Abale ace ndipo anati kwa iye, Kodi udzakhala mfumu yathu ndithu? kapena udzatilamulira ife ndithu kodi? ndipo anamuda Iye koposa cifukwa ca maloto ace ndi mau ace.
9 Ndipo analotanso lata lina, nafotokozera abale ace, nati, Taonani, ndalotanso lata lina: ndipo taonani, dzuwa ndi mwezi ndi nyenyezi khumi ndi imodzi zinandiweramira ine.
10 Ndipo iye anafotokozera atate wace ndi abale ace; ndipo atate wace anamdzudzula, nati kwa iye, Loto limene walota iwe nlotani? Kodi ine ndi amai ako ndi abale ako tidzafika ndithu tokha kuweramira iwe pansi?
11 Ndipo abale ace anamcitira iye nsanje, koma atate wace anasunga mau amene m'mtima mwace.
12 Ndipo abale ace ananka kukaweta zoweta za atate wao m'Sekemu.
13 Ndipo Israyeli anati kwa Yosefe, Kodi abale ako sadyetsa zoweta m'Sekemu? tiyeni, ndikutuma iwe kwa iwo. Ndipo anati, Ndine pano.
14 Ndipo anati kwa iye, Pita tsopano, nukaone ngati abale ako ali bwino, ndi ngati zoweta ziri bwino; nundibwezere ine mau. Ndipo anamtuma iye kucokera m'cigwa ca Hebroni, ndipo anadza ku Sekemu.
15 Ndipo anampeza munthu, taonani, analinkusokera m'thengo; munthuyo ndipo anamfunsa, nati, Kodi ufuna ciani?
16 Ndipo iye anati, Ndifuna abale anga. Undiuzetu kumene adyetsa zoweta.
17 Munthuyo ndipo anati, Anacoka pano; pakuti ndinamva alinkuti, Timuke ku Dotana. Yosefe ndipo anatsata abale ace, nawapeza ali ku Dotana.
18 Ndipo iwo anamuona iye ali patari, ndipo asanayandikire pafupi ndi iwo, anampangira iye ciwembu kuti amuphe.
19 Ndipo anati wina ndi mnzace, Taonani, alinkudza mwini maloto uja.
20 Tiyeni tsopano timuphe iye timponye m'dzenje, ndipo tidzati, Wajiwa ndi cirombo; ndipo tidzaona momwe adzacita maloto ace.
21 Ndipo Rubeni anamva nampulumutsa iye m'manja mwao; nati, Tisamuphe iye,
22 Ndipo Rubeni anati kwa iwo, Musakhetse mwazi; mponyeni iye m'dzenjemo m'cipululu muno, koma musamsamulire iye manja: kuti ampulumutse iye ra'manja mwao, ambwezenso kwa atate wace.
23 Ndipo panali pamene Yosefe anafika kwa abale ace, anambvula Yosefe malaya ace, malaya amwinjiro amene anabvala iye;
24 ndipo anamtenga iye, namponya m'dzenjemo; m'dzenjemo munalibe kanthu, munalibe madzi m'menemo.
25 Ndipo iwo anakhala pansi kuti adye cakudya; ndipo anatukula maso ao, nayang'ana, ndipo taonani, ulendo wa Aismayeli anacokera ku Gileadi ndi ngamila zao, zilinkunyamula zonunkhira ndi mafuta amankhwala ndi libano alinkumuka kutsikira nazo ku Aigupto.
26 Ndipo Yuda anati kwa abale ace, Nanga tidzapindulanji tikamupha mbale wathu ndi kufotsera mwazi wace?
27 Tiyeni timgulitse iye kwa Aismayeli, tisasamulire iye manja; cifukwa ndiye mbale wathu, thupi lathu. Ndipo anamvera iye abale ace.
28 Ndipo ana pita pamenepo Amidyani a malonda: ndipo anamturutsa namkweza Yosefem'dzenjemo, namgulitsa kwa Aismayeli ndi ndalama zasiliva makumi awiri; ndipo ananka naye Yosefe ku Aigupto.
29 Ndipo Rubeni anabwera kudzenje, ndipo taonani, Yosefe mulibe m'dzenjemo: ndipo iye anang'amba nsaru yace.
30 Ndipo anabwera kwa abale ace, nati, Mwana palibe; ndipo ine ndipita kuti?
31 Ndipo anatenga malaya ace a Yosefe, napha tonde, nabvika malaya m'mwazi wace:
32 natumiza malaya amwinjiro, nadza nao kwa atate ao: ndipo anati, Siwa tawatola; muzindikire tsono ngati ndi malaya a mwana wanu, kapena ndi ena.
33 Ndipo anazindikira nati, Ndiwo malaya a mwana wanga: wajiwa ndi cirombo: Yosefe wakadzulidwa ndithu.
34 Yakobo ndipo anang'amba malaya ace, nabvala ciguduli m'cuuno mwace namlirira mwana wace masiku ambiri.
35 Ndipo ana amuna ace onse ndi ana akazi onse anauka kuti amtonthoze: koma anakana kutonthozedwa; ndipo anati, Pakuti ndidzatsikira kumanda kwa mwana wanga, ndirinkulirabe. Atate wace ndipo anamlirira.
36 Amidyani ndipo anamgulitsa iye anke ku Aigupto kwa Potifara, nduna ya Farao, kazembe wa alonda.
1 Ndipo panali nthawi yomweyo, kuti Yuda anatsikira kwa abale ace nalowa kwa M-adulami, dzina lace Hira.
2 Ndipo Yuda anaona kumeneko mwana wamkazi wa Mkanani dzina lace Sua: ndipo anamtenga, nalowa kwa iye.
3 Ndipo anatenga pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Eri.
4 Ndipo anatenganso pakati, nabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Onani.
5 Ndipo anabalanso mwana wamwamuna, namucha dzina lace Sela: ndipo iye anali pa Kezibi pamene mkazi anambala iye,
6 Ndipo Yuda anamtengera Eri mwana wace woyamba mkazi, ndipo dzina lace ndilo Tamara.
7 Koma Eri mwana wace woyamba wa Yuda anali woipa pamaso pa Yehova: ndipo Yehova anamupha iye.
8 Ndipo Yuda anati kwa Onani, Lowani naye mkazi wa mbale wako, ndi kumcitira mkazi zoyenera mphwace wa mwamuna wace, ndi kumuukitsira mkuru wako mbeu.
9 Ndipo Onani anadziwa kuti mbeu siidzakhala yace: ndipo panali pamene iye analowana naye mkazi wa mbale wace, kuti anaitaya pansi, kuti angampatse mbeu kwa mkuru wace.
10 Koma cimene iye anacita cinali coipa pamaso pa Mulungu, ndipo anamupha iyenso.
11 Ndipo Yuda anati kwa Tamara mpengozi wace, Khala wamasiye m'nyumba ya atate wako, kufikira akakula msinkhu Sela mwana wanga wamwamuna; cifukwa anati kuti, Angafe iyenso monga abale ace. Ndipo Tamara ananka nakhala m'nyumba ya atate wace.
12 Atacuruka masiku mwana wamkazi wa Sua, mkazi wace wa Yuda anafa; ndipo Yuda anatonthola mtima, nakwera kunka kwa akusenga nkhosa zace ku Timna, iye ndi bwenzi lace Hira, M-adulami.
13 Ndipo anamuuza Tamara, kuti, Taona, mpongozi wako akwera kunka ku Timna kuti akasenge nkhosa zace.
14 Pamenepo anabvula zobvala zacezamasiye, nadzipfundandi copfunda cace, nabvala nakhala pa cipata ca Enaimu, cifukwa ciri pa njira ya ku Timna; pakuti anaona kuti Sela anakula msinkhu, ndipo sanampatsa iye kuti akhale mkazi wace.
15 Pamene Yuda anamuona iye, anaganizira kuti ali mkazi wadama: cifukwa iye anabisa nkhope yace.
16 Ndipo iye anapatukira kwa mkazi panjira, nati, Tiyetu, ndilowane nawe; cifukwa sanamdziwa kuti ndiye mpongozi wace. Ndipo anati, Kodi udzandipatsa ine ciani kuti ulowane ndi ine.
17 Ndipo iye anati, Ndidzatumiza kwa iwe kamwana ka mbuzi ka m'ziweto. Ndipo mkazi nati, Kodi udzandipatsa ine cikole mpaka ukatumiza?
18 Ndipo iye anati, Cikole canji ndidzakupatsa iwe? Ndipo mkazi anati, Mphete yako, ndi cingwe cako, ndi ndodo iri m'dzanja lako. Ndipo anampatsa izo, nalowana naye, ndipo mkazi anatenga pakati ndi iye.
19 Ndipo mkazi anauka nacoka, nabvula copfunda cace, nabvala zobvala zamasiye zace.
20 Ndipo Yuda anatumiza kamwana ka mbuzi ndi dzanja la bwenzi lace Madulami, kuti alandire cikole pa dzanja la mkazi; koma sanampeza iye.
21 Ndipo anafunsa amuna a pamenepo kuti, Ali kuti wadama uja anali pambali pa njira pa Enaimu? ndipo iwo anati, Panalibe wadama pano.
22 Ndipo iye anabwera kwa Yuda nati, Sitinampeza mkazi; ndiponso amuna a pamenepo anati, Panalibe wadama pano.
23 Ndipo Yuda anati, Azilandire kuti tingacitidwe manyazi: taona, ndinatumiza mwana uyu wa mbuzi, ndipo sunampeza iye.
24 Ndipo panali itapita miyezi itatu, anamuuza Yuda kuti, Tamara mpongozi wako wacita cigololo, ndiponso taonani, ali ndi pakati ndi cigololoco. Ndipo Yuda anati, Mturutse iye kuti amponye pamoto.
25 Pamene anamturutsa Iye, mkazi anatumiza kwa mpongozi wace kuti, Ndi mwamuna mwini izi ndatenga pakati; ndipo mkazi anati, Tayang'anatu, za yani zimenezi, mphete, ndi cingwe, ndi ndodo?
26 Ndipo Yuda anabvomereza nati, Akhale wolungama wopambana ine, cifukwa ine sindinampatsa iye Sela mwana wanga wamwamuna. Ndipo iye sanamdziwanso mkaziyo.
27 Ndipo panali nthawi ya kubala kwace, taonani, amapasa anali m'mimba mwace.
28 Ndipo panali pamene anabala kuti mmodzi anaturutsa dzanja; ndipo namwino anatenga cingwe cofiira namanga pa dzanja lace, kuti, Uyu anayamba kubadwa.
29 Ndipo panali pamene iye ana bweza dzanja lace, kuti, taona, mbale wace anabadwa, ndipo namwino anati, Wadziposolera wekha bwanji? cifukwa cace dzina lace linachedwa Pereze.
30 Ndipo pambuyo pace anabadwa mbale wace, amene anali ndi cingwe cofiira pamkono pace, dzina lace linachedwa Zera.
1 Ndipo anatsika naye Yosefe kunka ku Aigupto; ndipo Potifara, nduna ya Farao, kazembe wa alonda, Maigupto, anamgula iye m'manja mwa Aismayeli amene anatsika naye kunka iumeneko.
2 Ndipo Yehova anali ndi Yosefe; ndipo iye anali wolemeralemera; nakhala m'nyumba ya mbuyace M-aigupto.
3 Ndipo mbuyace anaona kuti Yehova anali ndi iye, ndi kuti Yehova anamlemereza m'dzanja lace zonse anazicita.
4 Ndipo Yosefe anapeza ufulu pamaso pace, ndipo anamtumikira iye; ndipo anamuyesa iye woyang'anira pa nyumba yace, naika m'manja mwace zonse anali nazo.
5 Ndipo panali ciyambire anamuyesa iye woyang'anira pa nyumba yace, ndi pa zace zonse, Yehova anadalitsa nyumba ya M-aigupto cifukwa ca Yosefe; ndipo mdalitso wa Yehova unali pa zace zonse, m'nyumba ndi m'munda.
6 Ndipo iye anasiya zace zonse m'manja a Yosefe; osadziwa comwe anali naco, koma cakudya cimene anadya. Ndipo Yosefe anali wokoma thupi ndi wokongola.
7 Ndipo panali zitapita izi, kuti mkazi wa mbuyace anamyang'anira maso Yosefe: ndipo mkaziyo anati, Gona ndi ine.
8 Koma iye anakana, nati kwa mkazi wa mbuyace, Taonani, mbuyanga sadziwa cimene ciri ndi ine m'nyumbamu, ndipo anaika zace zonse m'manja anga;
9 mulibe wina m'nyumba wamkuru ndine; ndipo sanandikaniza ine kanthu, koma iwe, cifukwa kuti uli mkazi wace: nanga ndikacita coipa cacikuru ici bwanji ndi kucimwira Mulungu?
10 Ndipo pali pakunenanena ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, iye sanamvera mkazi kugona naye kapena kukhala naye.
11 Ndipo panali, nthawi yomweyo, iye analowa m'nyumba kuti agwire nchito yace; ndipo munalibe amuna a m'nyumba m'katimo.
12 Ndipo mkazi anagwira iye copfunda cace, nati, Gona ndi ine; ndipo anasiya copfunda cace m'dzanja lace nathawa, naturukira kubwalo.
13 Ndipo panali pamene mkazi anaona kuti anasiya copfunda cace m'dzanja lace, nathawira kubwalo,
14 anaitana amuna a m'nyumba yace, nanena ndi iwo kuti, Taonani, walowetsa kwa ife Mhebri kuti atiseke ife, analowa kwa ine kugona ndi ine, ndipo ndinapfuula ndi mau akuru:
15 ndipo panali pamene iye anamva kuti ndinakweza mau anga ndi kupfuula, iye anasiya copfunda cace kwa me nathawira kubwalo.
16 Ndipo anasunga copfunda cace cikhale ndi iye kufikira atabwera kwao mbuyace.
17 Ndipo ananena kwa iye monga mau awa, nati, Analowa kwa ine kapolo wa Cihebri uja, munabwera naye kwathu, kundipunza ine:
18 ndipo panali pamene ndinakweza mau anga ndi kupfuula, iye anasiya cobvala cace kwa ine, nathawira kunja.
19 Ndipo panali pamene mbuyace anamva mau a mkazi wace, amene ananena kwa iye, kuti, Coteroci anandicitira ine kapolo wako; kuti iye anapsya mtima.
20 Ndipo mbuyace wa Yosefe anamtenga iye namuika m'kaidi, umo anamangidwa akaidi a mfumu: ndipo iye anali m'mwemo m'kaidimo.
21 Koma Yehova anali ndi Yosefe namcitira iye zokoma, nampatsa ufulu pamaso pa woyang'anira kaidi.
22 Ndipo woyang'anira kaidi anapereka m'manja a Yosefe akaidi onse okhala m'kaidimo, ndipo zonse iwo anazicita m'menemo, iye ndiye wozicita.
23 Woyang'anira m'kaidi sanayang'anira kanthu kali konse kamene kanali m'manja a Yosefe, cifukwa Yehova anali ndi iye; ndipo zimene anazicita, Yehova anazipindulitsa.
1 Ndipo panali zitapita izi, wopereka cikho wa mfumu ya Aigupto ndi wophika mkate wace anamcimwira mbuye wao mfumu ya Aigupto.
2 Ndipo Farao anakwiyira akuru ace awiriwo wamkuru wa opereka cikho, ndi wamkuru wa ophika mkate.
3 Ndipo anaika iwo asungidwe m'nyumba ya kazembe wa alonda, m'kaidi, umo anamangidwa Yosefe.
4 Ndipo kazembe wa alonda anapereka iwo kwa Yosefe, ndipo iye anawatumikira iwo: ndipo anakhala nthawi mosungidwamo.
5 Ndipo analota maloto onse awiri, yense lata lace, usiku umodzi, yense monga mwa kumasulira kwa loto lace, wopereka cikho ndi wophika mkate wa mfumu ya Aigupto, amene anamangidwa m'kaidi.
6 Ndipo Yosefe analowa kwa iwo m'mawa, nawaona iwo, taonani, anali oziya.
7 Ndipo anafunsa akuru a Farao osungidwa naye m'nyumba ya mbuyace, kuti, Nkhope zanu zagwa bwanji lero?
8 Ndipo iwo anati kwa iye, Ife talota maloto, ndipo tiribe wotimasulira. Ndipo Yosefe anati kwa iwo, Kodi Mwini kumasulira si ndiye Mulungu? Mundifotokozeretu.
9 Ndipo wopereka cikho wamkuru anafotokozera Yosefe loto lace, nati kwa iye, M'kulota kwanga, taona, mpesa unali pamaso panga:
10 ndipo m'mpesamo munali nthambi zitatu: ndipo unali wonga unaphuka, ndipo maluwa ace anaphuka; nabala matsamvu ace mphesa zakuca:
11 ndipo cikho ca Farao cinali m'dzanjalanga: ndipo ndinatenga mphesa, ndi kufinyira m'cikho ca Farao ndi kupereka cikho m'dzanja la Farao.
12 Ndipo Yosefe anati kwa iye, Mmasuliro wace ndi uwu: nthambi zitatu ndizo masiku atatu;
13 akali masiku atatu Farao adzatukula mutu wako, nadzabwezera iwe nchito yako; ndipo udzapereka cikho ca Farao m'dzanja lace, monga kale lomwe m'mene unali wopereka cikho cace.
14 Koma undikumbukire ine m'mene kudzakhala bwino ndi iwe, ndipoundicitiretu ine kukoma mtima: nundichule ine kwa Farao, nunditurutse ine m'nyumbamu:
15 cifukwa kuti ndinabedwa ndithu m'dziko la Ahebri; ndiponso pano sindinacite kanthu kakundiikira ine m'dzeniemu.
16 Pamene wophika mkate anaona kuti mmasuliro wace unali wabwino, iye anati kwa Yosefe, Inenso ndinalimkulota, ndipo, taonani, malicero atatu a mikate yoyera anali pamtu panga;
17 m'licelo lapamwamba munali mikate ya Farao ya mitundu mitundu; ndipo mbalame zinadya ya m'licelo la pamutu panga.
18 Ndipo Yosefe anayankha nati, Mmasuliro wace ndi uwu: malicelo atatu ndiwo masiku atatu;
19 akali masiku atatu Farao adzakweza mutu wako ndi kuucotsa, nadzakupacika iwe pamtengo: ndipo mbalame zidzadya mnofu wako.
20 Ndipo panali tsiku lacitatu ndilo tsiku lakubadwa kwace kwa Farao, iye anakonzera anyamata ace madyerero, ndipo anakweza mutu wa wopereka cikho wamkuru, ndi mutu wa wophika mkate wamkuru pakati pa anyamata ace.
21 Ndipo anabwezanso wopereka cikho ku nchito yace; ndipo iye anapereka cikho m'manja a Farao.
22 Koma anampacika wophika mkate wamkuru; monga Yosefe anawamasulira.
23 Koma wopereka cikho wamkuru sanakumbukira Yosefe, koma anamuiwala.
1 Ndipo panali zitapita zaka ziwiri zamphumphu, Farao analota; ndipo, taonani, anaima panyanja.
2 Ndipo, taonani, zinaturuka m'nyanja ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri za maonekedwe okoma ndi zonenepa; ndipo zinadya mabango.
3 Ndipo, taonani ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zinaturuka m'nyanjamo pambuyo pao, za maonekedwe oipa ndi zoonda; ndipo zinaima pa ng'ombe zinazo m'mphepete mwa nyanja.
4 Ndipo ng'ombe zazikazi za maonekedwe oipa ndi zoonda zinadya ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri za maonekedwe abwino ndi zonenepazo. Ndipo Farao anauka.
5 Ndipo anagona nalotanso kaciwiri: ndipo taonani, ngala zisanu ndi ziwiri za tirigu zinamera pa mbuwa imodzi, zonenepa ndi zabwino.
6 Ndipo, taonani, ngala zisanu ndi ziwiri, zoonda zopsyerera ndi mphepo ya kum'mawa, zinamera pambuyo pao.
7 Ndipo ngala zoondazo zinameza ngala zisanu ndi ziwiri zonenepa ndi zodzalazo. Ndipo Farao anauka, ndipo, taonani, analota.
8 Ndipo panali m'mamawa mtima wace unabvutidwa; ndipo anatumiza naitana amatsenga onse a m'Aigupto, ndi anzeru onse a momwemo: ndipo Farao anafotokozera iwo loto lace; koma panalibe mmodzi anakhoza kuwamasulira iwo kwa Farao.
9 Pamenepo wopereka cikho wamkuru anati kwa Farao, kuti, Ine ndidzakumbukira zocimwa zanga lero.
10 Farao anakwiya ndi anyamata ace, nandiika ine ndisungidwe m'nyumba ya kazembe wa alonda, ine ndi wophika mkate wamkuru:
11 ndipo tinalota loto usiku umodzi ine ndi iye; tinalota munthu yense monga mwa kumasulira kwa loto lace.
12 Ndipo panali ndi ife mnyamata, Mhebri, kapolo wa kazembe wa alonda, ndipo ife tinafotokozera iye, ndipo iye anatimasulira ife maloto athu; kwa munthu yense monga mwa loto lace anatimasulira.
13 Ndipo panali monga momwe iye anatimasulira, momwemo mudacitika; ine anandibwezera mu utumiki wanga, mnzanga anampacika.
14 Ndipo Farao anatumiza nakaitana Yosefe; ndipo anamturutsa iye msanga m'dzenjemo: ndipo iye anameta, napindula malaya ace, nalowa kwa Farao.
15 Farao ndipo anati kwa Yosefe, Ine ndalota loto, koma palibe wondimasulira; ndipo ndamva alikunena za iwe kuti, ukamva loto udziwa kumasulira.
16 Ndipo Yosefe anayankha Farao kuti, Si mwa ine; koma Mulungu adzayankha Farao mwamtendere.
17 Ndipo Farao ananena kwa Yosefe, M'loto langa taona, ndinaima m'mphepete mwa nyanja;
18 ndipo taona, zinaturuka m'nyanjamo ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri, zonenepa ndi za maonekedwe abwino; ndipo zinadya m'mabango;
19 ndipo, taona, ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zina zinaturuka pambuyo pao zosauka ndi za maonekedwe oipa ndi zoonda, zoipa zotere sindinazione m'dziko la Aigupto;
20 ndipo ng'ombe zazikazi zoonda ndi za maonekedwe oipa zinadya ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zonenepa,
21 Ndipo pamene zinadya sizinadziwika kuti zinadya; koma zinaipabe m'maonekedwe ao monga poyamba.
22 Pamenepo ndinauka. Ndipo ndinaona m'kulota kwanga, taona, ngala zisanu ndi ziwiri zinamera pa mbuwa imodzi zodzala ndi zabwino;
23 ndipo, taona, ngala zisanu ndi ziwiri zina zofota, zoonda, zopsyerera ndi mphepo ya kum'mawa, zinamera pambuyo pao;
24 ndipo ngala zoonda zinameza ngala zisanu ndi ziwiri zabwino; ndipo ndinafotokozera amatsenga: koma panalibe wondimasulira ine.
25 Ndipo Yosefe anati kwa Farao, Loto la Farao liri limodzi: cimene Mulungu ati acite wammasulira Farao.
26 Ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zabwino ndizo zaka zisanu ndi ziwiri, ndi ngala zisanu ndi ziwiri zabwino ndizo zaka zisanu ndi ziwiri: loto liri limodzi.
27 Ng'ombe zazikazi zisanu ndi ziwiri zoonda ndi za maonekedwe oipa zinaturuka pambuyo pao ndizo zaka zisanu ndi ziwiri, ndiponso ngala zisanu ndi ziwiri zopanda kanthu zopsyerera ndi mphepo ya kum'mawa, ndizo zaka zisanu ndi ziwiri za njala.
28 Ici ndi cinthu cimene ndinena kwa Farao: cimene Mulungu ati acite wasonyeza kwa Farao.
29 Taonani, zidzafika zaka zisanu ndi ziwiri zakucuruka cakudya m'dziko lonse la Aigupto;
30 ndipo pambuyo pao zidzauka zaka zisanu ndi ziwiri za njala; ndipo anthu adzaiwala zocuruka zonsezo m'dziko la Aigupto; ndipo njala idzapululutsa dziko;
31 ndipo zocuruka sizidzazindikirika cifukwa ca njala ikudza m'mbuyoyo, pakuti idzabvuta.
32 Ndipo lotolo linabwezedwa kawiri kwa Farao, cifukwa cinthu ciri cokhazikika ndi Mulungu, ndipo Mulungu afulumira kucicita.
33 Tsopano, Farao afunefune'munthu wakuzindikira ndi wanzeru, amkhazike iye ayang'anire dziko la Aigupto.
34 Farao acite cotere, alembe woyang'anira dziko wosonkhetsa limodzi la magawo asanu la dziko la Aigupto m'zaka zisanu ndi ziwiri zakucuruka dzinthu.
35 Iwo asonkhanitse cakudya conse ca zaka zabwino izo zirinkudzazo, aunjike tirigu m'manja a Farao akhale cakudya m'midzi, namsunge.
36 Ndipocakudyacocidzakhalam'dziko cosonkhera zaka zisanu ndi ziwiri za njala imene idzakhala m'dziko la Aigupto; kuti dziko lisanonongedwe ndi njala.
37 Ndipo cinthuco cinali cabwino m'maso mwa Farao, ndi m'maso mwa anyamata ace.
38 Ndipo Farao anati kwa anyamata ace, Kodi ife tidzaone munthu ngati uyu, mzimu wa Mulungu uli m'mtima mwace?
39 Ndipo Farao anati kwa Yosefe, Popeza Mulungu wakuonetsa iwe zonsezo palibe wina wakuzindikira ndi wanzeru ngati iwe.
40 Uziyang'anira pa nyumba yanga, ndipo anthu anga onse adzalamulidwa mwa mau ako; pa mpando wacifumu pokha ine ndidzakuposa iwe.
41 Ndipo Farao anati kwa Yosefe, Taona, ndakhazika iwe wolamulira dziko lonse la Aigupto.
42 Ndipo Farao anacotsa mphete yosindikizira yace pa dzanja lace, naibveka pa dzanja la Yosefe, nambveka iye ndi zobvalira zabafuta, naika unyolo wagolidi pakhosi pace;
43 ndipo anamkweza iye m'gareta wace waciwiri amene anali naye: ndipo anapfuula patsogolo pa iye, Gwadani; ndipo anamkhazika iye wolamulira dziko lonse la Aigupto,
44 Ndipo Farao anati kwa Yosefe, Ine ndine Farao, ndipo popanda iwe palibe munthu ali yense adzatukula dzanja lace kapena mwendo wace m'dziko lonse la Aigupto.
45 Ndipo Farao anamucha dzina la Yosefe Zafenati-Panea; ndipo anampatsa akwatire Asenati mwana wamkazi wa Potifera wansembe wa Oni. Ndipo Yosefe anaturuka wolamulira, nayendayenda m'dziko la Aigupto.
46 Ndipo Yosefe anali wa zaka makumi atatu pamene iye anaima pamaso pa Farao mfumu ya Aigupto, Ndipo Yosefe anaturuka pamaso pa Farao, napitapita pa dziko lonse la Aigupto,
47 Ndipo zaka zisanu ndi ziwiri zakucuruka dzinthu nthaka inabala zambirimbiri.
48 Ndipo anasonkhanitsa cakudya conse ca zaka zisanu ndi ziwiri cimene cinali m'dziko la Aigupto, nasunga cakudyaco m'midzi; cakudya ca m'minda, yozinga midzi yonse, anacisunga m'menemo.
49 Ndipo Yosefe anasunga tirigu ngati mcenga wa panyanja, wambirimbiri kufikira analeka kuwerenga; cifukwa anali wosawerengeka.
50 Ndipo kwa Yosefe anabadwa ana amuna awiri, cisanafike caka ca njala, amene Asenati mwana wamkazi wa Porifera wansembe wa Oni anambalira iye.
51 Ndipo Yosefe anamucha dzina la woyamba Manase, cifukwa anati iye, Mulungu wandiiwalitsa ine zobvuta zanga zonse, ndi nyumba yonse ya atate wanga.
52 Ndipo dzina la waciwiri anamucha Efraimu: cifukwa Mulungu anandibalitsa ine m'dziko la kusauka kwanga.
53 Ndipo zaka zakucuruka dzinthu zisanu ndi ziwiri za m'dziko la Aigupto, zinatha.
54 Ndipo zinayamba kufika zaka zisanu ndi ziwiri za njala, monga ananena Yosefe; ndipo munali njala m'maiko monse; koma m'dziko lonse la Aigupto munali cakudya.
55 Ndipo pamene dziko lonse la Aigupto linali ndi njala, anthu anapfuulira Farao awapatse cakudya; ndipo Farao anati kwa Aaigupto onse, Pitani kwa Yosefe: cimene iye anena kwa inu citani.
56 Ndipo njala inali pa dziko lonse lapansi; ndipo Yosefe anatsegula nkhokwe zonse nagulitsa Aaigupto: ndipo njala inakula m'dziko la Aigupto.
57 Ndipo maiko onse anafika ku Aigupto kudzagula tirigu kwa Yosefe: cifukwa njala inakula m'dziko lonse lapansi.
1 Ndipo anaona Yakobo kuti m'Aigupto munali tirigu, nati Yakobo kwa ana ace amuna, Cifukwa canji mulinkuyang'anana?
2 Ndipo iye anati, Taonani, ndamva kuti m'Aigupto muli tirigu, mutsikireko mutigulire kumeneko; kuti tikhale ndi moyo, tisafe.
3 Ndipo abale ace a Yosefe khumi anatsikira kukagula tirigu m'Aigupto.
4 Koma Yakobo sanamtuma Benjamini mphwace wa Yosefe, pamodzi ndi abale ace, cifukwa anati, Coipa cingamgwere iye.
5 Ndipo ana amuna a Israyeli anadza kudzagula mwa iwo amene anadzako, pakuti m'dziko la Kanani munali njala.
6 Ndipo Yosefe anali wolamulira dziko; ndiye amene anagulitsa kwa anthu onse a m'dziko; ndipo anafika abale ace a Yosefe, namweramira pansi, nkhope zao pansi.
7 Ndipo Yosefe anaona abale ace, ndipo anazindikira iwo, koma anadziyesetsa kwa iwo ngati mlendo, nanena kwa iwo mwankhanza: ndipo anati kwa iwo, Mufuma kuti inu? nati iwo, Ku dziko la Kanani kudzagula cakudya.
8 Ndipo Yosefe anazindikira abale ace, koma iwo sanamzindikira iye.
9 Ndipo Yosefe anakumbukira maloto amene analoto za iwo, ndipo anati kwa iwo, Ozonda inu; mwadzera kudzaona usiwa wa dziko.
10 Ndipo iwo anati kwa iye, Iai, mbuyanga, koma akapolo anu adzera kudzagula cakudya.
11 Tonse tiri ana amuna a munthu mmodzi; tiri oona, akapolo anu, sitiri ozonda.
12 Ndipo iye anati kwa iwo, Iai, koma mwadzera kuti muone usiwa wa dziko.
13 Nati iwo, Akapolo anu ndife abale khumi, ana amuna a munthu mmodzi m'dziko la Kanani; ndipo, taonani, wamng'ono ali ndi atate wathu lero; ndipo palibe mmodzi.
14 Ndipo Yosefe anati kwa iwo, dico cimene ndinakunenani inu, kuti, Ndinu ozonda.
15 Mudzayesedwa ndi ici, pali moyo wa Farao, simudzaturuka muno, koma akadze kuno mphwanu ndiko.
16 Tumizani mmodzi wa inu akatenge, adze naye mphwanu: ndipo inu mudzamangidwa kuti mau anu ayesedwe, ngati zoona ziri mwa inu: penatu, pali moyo wa Farao, muli ozonda ndithu.
17 Ndipo anaika onse m'kaidi masiku atatu.
18 Ndipo Yosefe anati kwa iwo tsiku lacitatu, Citani ici, kuti mukhale ndi moyo; ine ndiopa Mulungu;
19 ngati muli oona, mmodzi wa abale anu amangidwe m'kaidi momwemo; mukani inu, mupite naye tirigu wa njala ya mabanja anu;
20 koma mukatenge mphwanu kudza naye kwa ine, kuti atsimikizidwe mau anu ndipo simudzafa. Ndipo anacita comweco.
21 Ndipo iwo anati wina ndi mnzace, Tacimwiratu mbale wathu, pamene tinaona kubvutidwa kwa mtima wace, potipembedzera ife, koma ife tinakana kumvera, cifukwa cace kubvutidwa kumene kwatifikira.
22 Ndipo Rubeni anayankha nati kwa iwo, Kodi sindinanena kwa inu kuti, Musacimwire mwanayu; ndipo inu munakana kumvera? cifukwa cacenso, taonani mwazi wace ufunidwa.
23 Ndipo sanadziwa kuti, Yosefe anamva; cifukwa anali ndi womasulira.
24 Ndipo anawafotokozera iwo nalira, nawatembenukiranso, nanena nao, nampatula Simeoni mwa iwo, nammanga iye pamaso pao.
25 Ndipo Yosefe analamulira kuti adzaze zotengera zao ndi tirigu, ndi kubweza ndalama zao, ali yense m'thumba mwace, ndi kuwapatsa phoso la panjira; ndipo anatero nao.
26 Ndipo anasenzetsa aburu ao tirigu wao nacokapo.
27 Ndipo pamene wina wa iwo anamasula thumba lace kuti adyetse buru wace pacigono, anapeza ndalama zace; taonani, zinali kukamwa kwa thumba lace.
28 Ndipo iye anati kwa abale ace, Wandibwezera ine ndalama zanga, taonani, ziri kukamwa kwa thumba langa; ndipo mitima yao inawadera iwo, nanthunthumira, natembenukirana wina ndi mnzace kuti, Nciani ici Mulungu waticitira ife?
29 Ndipo anadza kwa Yakobo atate wao ku dziko la Kanani, namfotokozera iye zonse zinaonekera kwa iwo;
30 kuti, Munthu mwini dziko, ananena ndi ife mwankharwe, natiyesa ife ozonda dziko.
31 Koma ife tinati kwa iye, Tiru anthu oona; sitiri ozonda;
32 tiri abale khumi ndi awiri, ana a atate wathu; wina palibe, ndipo lero wamng'ono ali ndi atate wathu m'dziko la Kanani.
33 Ndipo munthuyo mwini dziko anati kwa ife, Momwemu ndidzadziwa kuti muli anthu oona; siyani mmodzi wa abale anu pamodzi ndi ine, tengani tirigu wa njala ya kwanu, mukani;
34 idzani naye mphwanu kwa ine, ndipo ndidzadziwa kuti simuli ozonda koma anthu oona: comweco ndidzakubwezerani inu mbale wanu, ndipo mudzacita malonda m'dziko muno.
35 Ndipo panali pamene analikukhuthula matumba ao, taonani, phukusi la ndalama la yense linali m'thumba lace; ndipo pamene iwo ndi atate ao anaona mapukusi a ndalama anaopa,
36 Ndipo Yakobo atate wao anati kwa iwo, Munandilanda ine ana; Yosefe palibe, Simeoni palibe, ndipo mudzacotsa Benjamini: zonse zimene zandigwera.
37 Ndipo Rubeni anati kwa atate wace, kuti, Muwaphe ana anga amuna awiri ndikapanda kumbweza iye kwa inu; mumpereke iye m'manja mwanga, ndipo ine ndidzambwezanso kwa inu.
38 Ndipo iye anati, Mwana wanga sadzatsikira ndi inu, cifukwa kuti mkuru wace wafa, ndipo watsala iye yekha; ngati coipa cikamgwera iye m'njira m'mene mupitamo, inu mudzatsitsira ndi cisoni imvi zanga kumanda.
1 Ndipo njala inakula m'dzikomo.
2 Ndipo panali pamene atatha kudya tirigu yense anatengayo ku Aigupto atate wao anati kwa iwo, Pitaninso, mukatigulire ife cakudya pang'ono.
3 Ndipo Yuda ananena ndi iye kuti, Munthu uja anatilimbitsira mau kuti, Simudzaonanso nkhope yanga, koma mphwanu akhale ndi inu ndiko.
4 Ngati mudzatuma mphwathu pamodzi ndi ife, tidzatsikira ndi kugulira inu cakudya.
5 Koma mukapanda kumtuma iye sititsika; pakuti munthu uja anati kwa ife, Simudzaona nkhope yanga, ngati mphwanu sali ndi inu.
6 Ndipo Israyeli anati, Cifukwa ninji munandicitira ine coipa cotero kuti munamuuza munthuyo muli ndi mphwanu?
7 Ndipo iwo anati, Munthuyo anafunsitsa za ife, ndi za abale athu, kuti, Atate wanu alipo? Kodi muli ndi mphwanu? ndipo tinamfotokozera iye monga mwa mau amenewo: ngati tinadziwa kuti iye adzati, Idzani naye mphwanu?
8 Ndipo Yuda anati kwa atate wace Israyeli, Mumtume mnyamata pamodzi ndi ine ndipo ife tidzanyamuka ndi kupita; kuti tikhale ndi moyo tisafe, ife ndi inu ndi ana athu ang'ono.
9 Ine ndidzakhala cikole, pa manja anga mudzamfunsa: ndikapanda kumbwezera kwa inu ndi kumuimitsa pamaso panu, cifukwa cace cidzakhala pa ine masiku onse:
10 pakuti tikadaleka kucedwa mwenzi tsopano titabwera kawiri.
11 Ndipo Israyeli atate wao anati kwa iwo, Ngati comweco tsopano citani ici: tengani zipatso za m'dziko muno m'zotengera zanu, mumtengere munthu uja mphatso, mafuta a mankhwala pang'ono, ndi uci pang'ono, zonunkhira ndi mure, ndi mfula, ndi katungurume;
12 nimutenge ndalama zowirikiza m'manja mwanu; ndipo ndalama zimene zinabwezedwa kukamwa kwa matumba anu mutengenso m'manja mwanu; kapena sanacita dala;
13 mutengenso mphwanu, nimuoyamuke, mupitenso kwa munthu uja:
14 Mulungu Wamphamvuyonse adzakupatsani inu cifundo pamaso pa munthu uja, kuti akumasulireni inu mbale wanu wina ndi Benjamini. Ndipo ine, ngati ndikhala wopanda ana, ndikhalatu.
15 Amunawo ndipo anatenga mphatso, natenga ndalama zowirikiza m'manja mwao, ndi Benjamini; ndipo ananyamuka ndi kutsikira ku Aigupto, naima pamaso pa Yosefe.
16 Ndipo pamene anaona Benjamini pamodzi nao, anati kwa tsanyumba wace, Lowa nao anthuwo m'nyumba, kaphere iwo, kakoozere, cifukwa anthuwo adzadya ndi ine usana uno.
17 Munthuyo anacita monga anamuuza Yosefe, ndipo munthuyo analowa nao anthuwo m'nyumba ya Yosefe.
18 Anthuwo ndipo anaopa, cifukwa analowezedwa m'nyumba ya Yosefe; nati, Cifukwa ca ndalama zila zinabwezedwa m'matumba athu nthawi yoyamba ija, ife tilowezedwa, kuti aone cifukwa ndi ife, atigwere ife, atiyese ife akapolo, ndi aburu athu.
19 Ndipo anayandikira kwa tsanyumba wa Yosefe, ndipo ananena ndi iye pa khomo la nyumba, nati,
20 Mfumu, tinatsikira ndithu nthawi yoyamba kudzagula cakudya:
21 ndipo panali pamene ife tinafika padgono, tinamasula matumba athu, ndipo taonani ndalama za yense zinali kukamwa kwa thumba lace, ndalama zathu mkulemera kwace; ndipo tabwera nazo m'manja mwathu.
22 Ndalama zina tatenga m'manja mwathu kuti tigule cakudya: sitimdziwa amene anaika ndalama zathu m'matumba athu.
23 Ndipo iye anati, Mtendere ukhale ndi inu, musaope; Mulungu wanu, ndi Mulungu wa atate wanu anakupatsani inu cum a m'matumba anu; ine ndinali nazo ndalama zanu. Pamenepo anawaturutsira Simeoni.
24 Ndipo munthuyo analowetsa anthu m'nyumba ya Yosefe, nawapatsa iwo madzi, natsuka mapazi ao, napatsa aburu ao cakudya.
25 Ndipo anakonzeratu mphatso asanafike Yosefe usana; cifukwa anamva kuti adzadya cakudya pamenepo.
26 Pamene Yosefe anadza kunyumba kwace, analowa nazo m'nyumba mphatso zinali m'manja mwao, namweramira iye pansi.
27 Ndipo anafunsa iwo za ubwino wao, nati, Kodi atate wanu ali ndi moyo? wokalamba uja amene nunanena uja: kodi alipo?
28 Ndipo iwo anati, Kapolo wanu atate wathu ili bwino, alipo. Ndipo anawerama, namgwadira iye.
29 Ndipo iye anatucula maso ace naona Benjamini mphwace, mwana wa amace, nati, Kodi uyu ndi mphwanu wamng'ono uja, amene munanena ndi ine uja? Ndipo iye anati, Mulungu akucitire we ufulu, mwana wanga.
30 Ndipo Yosefe anafulumira, cifukwa mtima wace unakhumbitsa mphwace, ndipo mafuna polirira; nalowa m'cipinda ace naliramo.
31 Ndipo anasamba ikhope yace, naturuka; ndipo anadziletsa, nati, Ikani cakudya.
32 Ndipo anamuikira iye cace pa yekha, ndi wo cao pa okha, ndi Aaigupto ikudya naye cao pa okha; cifukwa aigupto sanathei kudya cakudya pamodzi ndi Ahebri: cifukwa kucita comweco nkunyansira Aaigupto.
33 Ndipo anakhala pamaso pace, woyanba monga ukuru wace, ndi wanng'ono mensa ung'ono wace; ndipo mazizwa wina ndi wina.
34 Ndipo mawagawira mitanda ya patsogolo pace; koma mtanda wa Benjamini maposa mitanda ya onsewo kasanu. Ndipo anamwa, nasekera pamodzi ndi iye.
1 Ndipo Yosefe anauza tsanyumba wace kuti, Dzaza matumba a anthuwo ndi cakudya, monga angathe kunyamula, ndi kuika ndalama za yense kukamwa kwa thumba lace.
2 Nuike cikho canga, cikho casiliva ciija, kukamwa kwa thumba la wamng'ono, pamodzi ndi ndalama za tirigu zace. Ndipo iye anacita monga mau ananena Yosefe.
3 Pamene kudaca, anamukitsa anthu iwo ndi aburu ao.
4 Ataturuka m'mudzi asanamuke patari, Yosefe anati kwa tsanyumba wace, Tanyamuka, talondola anthu aja, ukawapeza unene nao, Cifukwa canji mwabwezera zoipa m'malo mwa zabwino?
5 Kodi si ndico comwera naco mbuyanga, naombeza ula naco? Mwacitira coipa pakutero.
6 Ndipo anapeza iwo, nanena nao mau omwewo.
7 Nati kwa iye, Bwanji mbuyanga anena mau otere? Ngati nkutheka kuti akapolo anu acite cotero?
8 Taonani, ndalama zija, tinazipeza kukamwa kwa matumba athu, tinazibwezanso kwa inu kuturuka m'dziko la Kanani; nanga bwanji tingabe m'nyumba ya mbuyanga kapena siliva kapena golidi?
9 iye wa akapolo anu ampeza naco afe, ndipo ifenso tidzakhala akapolo a mbuyanga.
10 Ndipo iye mati, Tsononso cikhale monga mwa nau anu: iye amene ampeza naco adzakhala kapolo wanga; ndipo inu nudzakhala opanda cifukwa.
11 Ndipo anafulumira natsitsa pansi zense thumba lace, namasula yense humba lace.
12 Ndipo iye anafunauna kuyambira pa wamkuru naleka pa wamng'ono; nacipeza cikho n'thumba la Benjamini:
13 ndipo anang'amba zobvala zao, nasenzetsa yense buru wace, nabwera kumuzi.
14 Yudanso ndi abale ace anadza cu nyumba ya Yosefe; ndipo iye ikali pamenepo; ndipo anagwa oansi patsogolo pace.
15 Ndipo losefe anati kwa iwo, Ici nciani nwacicita? Kodi simudziwa kuti nunthu ngati ine ndingathe kuzindidra ndithu?
16 Ndico Yuda anati, Kodi tidzati bwanji kwa mbuyanga? kodi tidzanenanji? kapena tidzawiringula ife bwanji? Mulungu wapeza mphulupulu ya akapolo anu; taonani, tiri akapolo a mbuyanga, ife ndi iye amene anampeza naco cikho m'dzanja lace.
17 Ndipo iye anati, Ngati kutheka kuti ndicite cotero! Munthu amene anampeza naco m'dzanja lace adzakhala kapolo wanga: koma inu, kazipitani ndi mtendere kwa atate wanu.
18 Ndipo Yuda anayandikira kwa iye nati, Mfumu, kapolo wanu aneneretu m'makutu a mbuyanga, mtima wanu usapse pokwiya ndi kapolo wanu; cifukwa muli ngati Farao.
19 Mbuyanga anafunsa akapolo ace kuti, Kodi muli ndi atate wanu kapena mbale wanu?
20 Ndipo tinati kwa mbuyanga, Tiri ndi atate, munthu wokalamba, ndi mwana wa ukalamba wace wamng'ono; mbale wace wafa, ndipo iye yekha watsala wa amace, ndipo atate wace amkonda iye.
21 Ndipo munati kwa akapolo anu, Munditengere iye, kuti ndimuone iye m'maso mwanga.
22 Ndipo ife tinati kwa mbuyanga, Mnyamata sangathei kumsiya atate wace; pakuti akamsiya atate wace, atate wace adzafa.
23 Ndipo munati kwa akapolo anu, Koma ngati mbale wanu safika pamodzi ndi inu, simudzaonanso konse nkhope yanga,
24 Ndipo panali titakwera kunka kwa kapolo wanus atate, wanga, tinamfotokozera iye mau a mbuyanga.
25 Ndipo atate wathu anati, Mupitenso mutigulire ife cakudya pang'ono.
26 Ndipo ife tinati, Sitingathe kupita; mphwathu wamng'ono akakhala ndi ife, pamenepo tidzapita; pakuti sitingaone nkhope ya munthu uja, mphwathu wamng'ono akapanda kukhala ndi ife.
27 Ndipo kapolo wanu atate wanga anati kwa ife, Inu mudziwa kuti mkazi wanga anandibalira ine ana amuna awiri;
28 wina anaturuka kwa ine ndipo ndinati, Zoonatu, wakadzulidwa; ndipo sindidzamuonanso iye;
29 ndipo ngati mukandicotsera ameneyonso, ndipo ngati cimgwera coipa, mudzanditsitsira ndi cisoni imvi zanga kumanda.
30 Cifukwa cace ndikafika kwa kapolo wanu atate wanga, ndipo mnyamata akapanda kukhala ndi ife; popeza moyo wace uli womangidwa ndi moyo wa mnyamatayo;
31 kudzakhala pakuona kuti mnyamatayo palibe, adzafa; ndipo akapolo anu adzamtsitsira ndi cisoni imvi za atate wathu kumanda.
32 Pakuti kapolo wanu anadziyesa cikole ca mnyamata pa atate wanga, kuti, Ndikapanda kumbwezeranso kwa inu, pamenepo ndidzakhala ndi cifukwa kwa atate wanga nthawi zonse.
33 Tsopanotu, mtumiki wanu akhale kapolo wa mbuyanga m'malo mwa mnyamata; mnyamatayo akwere pamodzi ndi abale ace.
34 Pakuti ndidzakwera bwanji kwa atate wanga, mnyamatayo akapanda kukhala ndi ine? ndingaone coipa cidzagwera atate wanga.
1 Ndipo Yosefe sanakhoza kudziletsa pamaso pa onse amene anaima naye: nati, Turutsa anthu onse pamaso panga. Ndipo panalibe munthu pamodzi ndi iye pamene Yosefe anadziululira yekha kwa abale ace.
2 Ndipo analira momveka, ndipo anamva Aaigupto, ndipo anamva a m'nyumba ya Farao.
3 Ndipo Yosefe anati kwa abale ace, Ine ndine Yosefe; kodi-akali ndi moyo atate wanga? Ndipo abale ace sanakhoza kumyankha iye; pakuti anabvutidwa pakumuona iye.
4 Ndipo Yosefe anati kwa abale ace, Muyandikiretu kwa ine; nayandikira. Ndipo iye anati, Ine ndine Yosefe mbale wanu, ine ndemwe munandigulitsa ndilowe m'Aigupto.
5 Tsopano musaphwetekwe mtima, musadzikwiyira inu nokha, kuti munandigulitsira ine kuno, pakuti Mulungu ananditumiza ine patsogolo panu kuti ndisunge moyo.
6 Zaka ziwirizi muli njala m'dziko muno; ndipo zatsala zaka zisanu, zopanda kulima kapena kusenga,
7 Ndipo Mulungu anatumiza ine patsogolo panu kuti ndikhazike inu mutsale m'dziko lapansi, ndi kusunga inu amoyo ndi cipulumutso cacikuru.
8 Ndipo tsopano sindinu amene munanditumiza ine ndifike kuno, koma Mulungu, ndipo anandiyesa ine atate wa Farao, ndi mwini banja lace lonse, ndi wolamulira dziko lonse la Aigupto.
9 Fulumirani, kwerani kunka kwa atate wanga, muti kwa iye, Cotere ati Yosefe mwana wanu, Mulungu wandiyesa ine mwini Aigupto lonse: tsikirani kwa ine, musacedwe.
10 Ndipo mudzakhala m'dziko la Goseni, mudzakhala pafupi ndi ine, inu ndi ana anu, ndi ana a ana anu, ndi nkhosa zanu, ndi zoweta zanu, ndi zonse muli nazo;
11 ndipo ndidzacereza inu komweko; pakuti zatsala zaka zisanu za njala; kuti mungafikire umphawi, inu ndi banja lanu, ndi onse muli nao.
12 Taonani, maso anu aona, ndi maso a mphwanga Benjamini, kuti ndi m'kamwa mwanga ndirikulankhula ndi inu.
13 Ndipo mudzafotokozera atate wanga za ulemerero wanga wonse m'Aigupto, ndi zonse mwaziona; ndipo muzifulumira ndi kutsitsira kuno atate wanga.
14 Ndipo anagwa pakhosi pace pa Benjamini, nalira; ndipo Benjamini nalira pakhosi pace.
15 Ndipo anampsompsona abale ace onse, nalilira iwo; ndipo pambuyo pace abale ace onse anaceza naye.
16 Ndipo mbiri yace inamveka m'nyumba ya Farao, kuti abale ace a Yosefe afika; ndipo inamkomera Farao, ndi anyamata ace.
17 Ndipo Farao anati kwa Yosefe, Nena ndi abale ako, Citani ici; senzetsani nyama zanu, ndi kupita kunka ku dziko la Kanani;
18 katengeni atate wanu ndi mabanja anu, nimudze kwa ine; ndipo ndidzakupatsani inu zabwino za dziko la Aigupto, ndipo mudzadya zonenepa za dzikoli.
19 Tsopano mwalamulidwa citani ici; muwatengere ana anu ndi akazi magareta a m'dziko la Aigupto; nimubwere naye atate wanu.
20 Musasamalire cuma canu; popeza zabwino za dziko lonse la Aigupto ndi zanu.
21 Ndipo ana a Israyeli anacita cotero: ndipo Yosefe anawapatsa iwo magareta monga analamulira Farao, nawapatsa phoso la panjira,
22 Onse anawapatsa yense zobvala zopindula; koma Benjamini anampatsa ndalama zasiliva mazana atatu ndi zobvala zopindula zisanu.
23 Kwa atate wace anatumiza zotere: aburu khumi osenza zinthu zabwino za m'Aigupto, ndi aburu akazi khumi osenza tirigu, ndi cakudya, ndi phoso la atate la panjira.
24 Ndipo anamukitsa abale ace, ndipo anacoka; ndipo anati kwa iwo, Musakangane panjira.
25 Ndipo anakwera kuturuka m'Aigupto, nafika ku dziko la Kanani kwa Yakobo atate wao.
26 Ndipo anamfotokozera iye kuti, Yosefe akali ndi moyo, ndipo alamulira m'dziko lonse la Aigupto, Pamenepo mtima wace unakomoka, pakuti sanawakhulupirira iwo.
27 Ndipo anamfotokozera iye mau onse a Yosefe amene ananena ndi iwo; ndipo pamene anaona magareta amene Yosefe anatumiza kuti amtengeremo, mtima wa Yakobo atate wao unatsitsimuka;
28 ndipo Israyeli anati, Cakwana; Yosefe mwana wanga akali ndi moyo; ndidzamuka ndikamuone iye ndisanafe.
1 Ndipo Israyeli anamuka ulendo wace ndi zonse anali nazo, nafika ku Beereseba, napereka nsembe kwa Mulungu wa Isake atate wace.
2 Ndipo Mulungu ananena kwa Israyeli, m'masomphenya a usiku, nati, Yakobo, Yakobo.
3 Nati iye, Ndine pano. Ndipo anati, Ine ndine Mulungu, Mulungu wa atate wako; usaope kunka ku Aigupto; pakuti pamenepo ndidzakusandutsa iwe mtundu waukuru;
4 Ine ndidzatsikira pamodzi ndi iwe ku Aigupto; ndipo Ine ndidzakubwezanso ndithu; ndipo Yosefe adzaika dzanja lace pamaso pako.
5 Ndipo Yakobo anacoka ku Beereseba, ndipo ana amuna a Israyeli anamnyamula Yakobo atate wao, ndi ana ao ang'ono, ndi akazi ao, m'magareta amene Farao anatumiza kuti amnyamule iye,
6 Ndipo anatenga ng'ombe zao ndi cuma cao anacipezam'dziko la Kanani, nadza ku Aigupto, Yakobo ndi mbeu zace zonse pamodzi ndi iye;
7 ana ace amuna, ndi zidzukulu zace zazimuna, ndi ana akazi ace, ndi zidzukulu zace zazikazi, ndi mbeu zace zonse anadza nazo m'Aigupto.
8 Maina a ana a Israyeli amene anadza m'Aigupto ndi awa: Yakobo ndi ana amuna ace: Rubeni mwana wamwamuna woyamba wa Yakobo.
9 Ndi ana amuna a Ruberu Hanoki, ndi Palu, ndi Hezroni, ndi Karmi.
10 Ndi ana amuna a Simeoni: Yemueli ndi Yamini, ndi Ohadi, ndi Yakini, ndi Zohari, ndi Sauli, mwana wamwamuna wa mkazi wa ku Kanani.
11 Ndi ana amuna a Levi: Gerisoni, Kohati, ndi Merai.
12 Ndi ana amuna a Yuda: Eri, ndi Onani, ndi Sela, ndi Perezi, ndi Zera; koma Eri ndi Onani anafa m'dziko la Kanani. Ndi ana amuna a Perezi ndiwo Hezroni ndi Hamuli.
13 Ndi ana amuna a Isakara: Tola ndi Puva, ndi Yabi, ndi Simroni.
14 Ndi ana amuna a Zebuloni: Seredi, ndi Eloni ndi Yaledi.
15 Amenewo ndi ana amuna a Leya, amene anambalira Yakobo m'Padanaramu, pamodzi ndi mwana wamkazi wace Dina; ana amuna ndi akazi onse: ndiwo anthu makumi atatu kudza atatu.
16 Ndi ana amuna a Gadi: Zifioni, ndi Hagi, ndi Suni, ndi Ezboni, ndi Eri, ndi Arodi, ndi Areli.
17 Ndi ana amuna a Aseri: Yimna, ndi Yisiva, ndi Yisivi, ndi Beriya, ndi Sera mlongo wao; ndi ana a Beriya: Hebere, ndi Maliki eli.
18 Amenewa ndi ana a Zilipa, amene Labani anampatsa Leya mwana wace wamkazi, amenewo anambalira Yakobo, anthu khumi ndi asanu ndi mmodzi.
19 Ana a Rakele mkazi wace wa Yakobo: Yosefe ndi Benjamini.
20 Kwa Yosefe kunabadwa m'dziko la Aigupto Manase ndi Efraimu, amene Asenati mwana wamkazi wa Potifera wansembe wa Oni anambalira iye.
21 Ndi ana amuna a Benjamini: Bela ndi Bekeri, ndi Asibeli, ndi Gera, ndi Namani, ndi Ehi ndi Rosi, Mupimu ndi Hupimu, ndi Aridi.
22 Amenewo ndi ana a Rakele, amene anabadwira Yakobo; anthu onse ndiwo khumi ndi anai.
23 Ndi ana amuna a Dani: Husimu.
24 Ndi ana amuna a Nafitali: Yazeeli, ndi Guni, ndi Yezera ndi Silemu.
25 Amenewa ndi ana a Biliha, amene Labani anampatsa Rakele mwana wace wamkazi, amenewo anambalira Yakobo; anthu onse ndiwo asanu ndi awiri.
26 Ndi anthu onse amene anadza ndi Yakobo m'Aigupto, amene anaturuka m'cuuno mwace, pamodzi ndi akazi a ana amuna a Yakobo ndiwo makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi mmodzi;
27 ndi ana amuna a Yosefe, amene anambadwira iye m'Aigupto ndiwo anthu awiri; anthu onse a mbumba ya Yakobo, amene analowa m'Aigupto anali makumi asanu ndi awiri.
28 Ndipo anatumiza Yuda patsogolo pace kwa Yosefe, amtsogolere kumuonetsa njira yomka ku Goseni: ndipo anafika ku dziko la Goseni.
29 Ndipo Yosefe anamanga gareta lace nakwera kunka kukakomana naye Israyeli atate wace, ku Goseni, ndipo anadzionetsera yekha kwa iye, nagwera pakhosi pace nakhala m'kulira pakhosi pace.
30 Ndipo Israyeli anati kwa Yosefe, Ndife tsopano, popeza ndaona nkhope yako, kuti ukali ndi moyo.
31 Ndipo Yosefe anati kwa abale ace, ndi kwa mbumba ya atate wace, Ndidzanka, ndikauze Farao, ndipo ndidzati kwa iye, Abale anga ndi mbumba ya atate wanga, amene anali m'dziko la Kanani, afika kwa ine;
32 ndipo anthuwo ali abusa cifukwa anakhala oweta ng'ombe; ndipo anadza ndi nkhosa zao ndi ng'ombe zao ndi zonse ali nazo.
33 Ndipo padzakhala pamene Farao adzaitana inu, nadzati, Nchito yanu njotani?
34 mudzati, Akapolo anu akhala oweta ng'ombe ciyambire ubwana wathu kufikira tsopano, ife ndi atate athu; kuti mukhale m'dziko la Goseni; a cifukwa abusa onse anyansira Aaigupto.
1 Ndipo Yosefe analowa nauza Farao nati, Atate wanga ndi abale anga, ndi nkhosa zao ndi ng'ombe zao, ndi zonse ali nazo, anacokera ku dziko la Kanani; ndipo, taonani, ali m'dziko la Goseni.
2 Ndipo mwa abale ace anatengako anthu asanu, nawaonetsa iwo kwa Farao.
3 Ndipo Farao anati kwa abale ace, Nchito yanu njotani? ndipo iwo anati kwa Farao, Akapolo anu ndi abusa, ife ndi atate athu.
4 Nati kwa Farao, Tafika kuti tikhale m'dzikomo; popeza palibe podyetsa zoweta za akapolo anu; pakuti njala yakula m'dziko la Kanani. Mulole tsopano akapolo anu akhale m'dziko la Goseni.
5 Ndipo Farao anati kwa Yosefe, Atate wako ndi abale ako afika kwa iwe;
6 dziko la Aigupto liri pamaso pako: uwakhazike atate wako ndi abale ako pa dera lokometsetsa la dziko; akhale m'dziko la Goseni; ndipo ngati udziwa anthu anzeru a mwa iwo, uwaike iwo ayang'anire ng'ombe zanga.
7 Ndipo Yosefe analowa naye Yakobo atate wace, namuika iye pamaso pa Farao; ndipo Yakobo anamdalitsa Farao.
8 Ndipo Farao anati kwa Yakobo, Masiku a zaka za moyo wanu ndi angati?
9 Ndipo Yakobo anati kwa Farao, Masiku a zaka za ulendo wanga ndi zaka zana limodzi kudza makumi atatu; masiku a zaka za moyo wanga ali owerengeka ndi oipa, sanafikire masiku a zaka za moyo wa makolo angam'masikua ulendowao.
10 Ndipo Yakobo anamdalitsa Farao, naturuka pamaso pa Farao.
11 Ndipo Yosefe anakhazika atate wace ndi abale ace, napatsa iwo pokhala m'dziko la Aigupto, m'dera lokometsetsa la m'dziko, m'dziko la Ramese, monga analamulira Farao.
12 Ndipo Yosefe anacereza atate wace ndi abale ace, ndi mbumba yonse ya atate wace ndi cakudya monga mwa mabanja ao.
13 Ndipo munalibe cakudya m'dziko lonse; pakuti njala inalimba kwambiri; cifukwa cace dziko la Aaigupto ndi dziko la Kanani unalefuka cifukwa ca njalayo.
14 Ndipo Yosefe anasonkhanitsa ndalama zonse anazipeza m'dziko la Aigupto ndi m'dziko la Kanani, za tirigu amene anagula; ndipo Yosefe anapereka ndalama ku nyumba ya Farao.
15 Ndipo zitatha ndalama zonse m'dziko la Aigupto ndi m'dziko la Kanani, Aaigupto onse anadza kwa Yosefe, nati, Mutipatse ife cakudya; tiferenji pamaso panu? zatsirizika ndalama.
16 Ndipo Yosefe anati, Mundipatse ng'ombe zanu: ndipo ndidzakupatsani inu mtengo wa ng'ombe zanu ngati ndalama zatsirizika.
17 Ndipo anadza nazo ng'ombe zao kwa Yosefe, ndipo Yosefe anapatsa iwo cakudya cosinthana ndi akavalo, ndi nkhosa, ndi ng'ombe, ndi aburu; ndipo anawadyetsa iwo ndi cakudya cosinthana ndi zoweta zao zonse caka cimeneco.
18 Citatha caka cimeneco, anadza kwa iye caka caciwiri, nati kwa iye, Sitibisira mbuyathu kuti ndalama zathu zonse zatha; ndipo zoweta za ng'ombe oza mbuyathu: palibe kanthu kotsala pamaso pa mbuyathu, koma matupi athu ndi maiko athu;
19 tiferenji pamaso panu, ife ndi dziko lathu? mutigule ife ndi dziko lathu ndi cakudya, ndipo ife ndi dziko lathu tidzakhala akapolo a Farao; ndipo mutipatse ife mbeu, kuti tikhale ndi moyo, tisafe, ndi kuti dziko lisakhale labwinja.
20 Ndipo Yosefe anamgulira Farao dziko lonse la Aigupto, cifukwa Aaigupto anagulitsa yense munda wace, cifukwa njala inakula pa iwo; ndipo dziko linakhala la Farao.
21 Tsono anthu, anasunthira iwo ku midzi kucokera kumphepete kwa malire a Aigupto kufikira kumphepete kwina kwace.
22 Koma dziko la ansembe lokha sanagule, cifukwa ansembe analandira gawo lao kwa Farao, nadya gawolo anawapatsa Farao; cifukwa cace sanagulitsa dziko lao.
23 Ndipo Yosefe anati kwa anthu, Taonani, ndamgulira Farao inu ndi dziko lanu lero lomwe, taonani, mbeu zanu sizi, mubzale m'dziko.
24 Ndipo padzakhala pakukunkha, muzipatsa limodzi la mwa magawo asanu kwa Farao, koma magawo anai ndi anu, mbeu za munda, ndi za cakudya canu, ndi ca ana anu ndi mabanja anu.
25 Ndipo iwo anati, Watipulumutsa miyoyo yathu; tipeze ufulu pamaso pa mbuyanga, ndipo tidzakhala akapolo a Farao.
26 Ndipo Yosefe analamulira lamulo la pa dziko la Aigupto kuukira lero, kuti Farao alandire limodzi la mwa magawo asanu; koma dziko la ansembe lokha silinakhala la Farao.
27 Ndipo Israyeli anakhala m'dziko la Aigupto, m'dziko la Goseni; nakhala nazo zaozao m'menemo, nabalana nacuruka kwambiri.
28 Ndipo Yakobo anakhala m'dziko la Aigupto zaka khumi mphambu zisanu ndi ziwiri; ndipo masiku a Yakobo zaka za moyo wace zinali zaka zana limodzi mphambu makumi anai kudza zisanu ndi ziwiri.
29 Ndipo nthawi inayandikira kuti Israyeli adzafa, ndipo anaitana Yosefe mwana wace wamwamuna, nati kwa iye, Ngati ndapeza ufulu pamaso pako, ikatu dzanja lako pansi pa ncafu yanga, nundicitire ine zabwino ndi zoona: usandiikatu ine m'Aigupto;
30 koma pamene ndidzagona ndi makolo anga, udzanditenge ine kuturuka m'dziko la Aigupto, ukandiike ine m'manda mwao. Ndipo iye anati, Ndidzacita monga mwanena.
31 Ndipo anati, Undilumbirire ine; namlumbirira iye. Ndipo Israyeli anawerama kumutu kwa kama.
1 Ndipo panali zitapita izi, anthu anati kwa Yosefe, Taonani, atate wanu wadwala: ndipo iye anatenga ana ace amuna awiri, Manase ndi Efraimu, apite naye.
2 Ndipo anthu anamuuza Yakobo nati, Taonani, mwana wanu Yosefe alinkudza kwa inu; ndipo Yakobo anadzilimbitsa, nakhala tsonga pakama.
3 Ndipo Yakobo anati kwa Yosefe, a Mulungu Wamphamvuyonse anaonekera kwa ine pa Luzi m'dziko la Kanani nandidalitsa ine, nati kwa ine,
4 Taona, ndidzakubalitsa iwe, ndidzakucurukitsa iwe, ndidzakusandutsa iwe khamu la anthu a mitundu; ndipo ndidzapatsa mbeu yako ya pambuyo pako dziko ili likhale laolao cikhalire.
5 Tsopano ana ako amuna awiri, amene anakubadwira iwe m'dziko la Aigupto, ndisanadze kwa iwe ku Aigupto, ndiwo anga; Efraimu ndi Manase, monga Rubeni ndi Simeoni, ndiwo anga.
6 Koma obala iwe udzawabala pambuyo pao, ndiwo ako; awaphe dzina la abale ao m'colowa cao.
7 Tsono ine, pamene ndinacokera ku Padani, Rakele anamwalira pambali panga m'dziko la Kanani m'njira, itatsala nthawi yaing'ono tisadafike ku Efrati; ndipo ndidamuika iye pamenepo pa njira ya ku Efrati (ndiwo Betelehemu).
8 Ndipo Israyeli anayang'ana ana amuna a Yosefe, nati, Ndani awa?
9 Ndipo Yosefe anati kwa atate wace, Amenewa ndi ana anga, amene Mulungu wandipatsa ine pano. Ndipo iye anati, Udze naotu kwa ine, ndipo ndidzawadalitsa.
10 Koma maso a Israyeli anali akhungu m'ukalamba wace, ndipo sanathei kuona. Ndipo anadza nao pafupi; ndipo anapsompsona iwo, nawafungatira.
11 Ndipo Israyeli anati kwa Yosefe, Sindinaganizira kuti ndione nkhope yako: ndipo, taona, Mulungu wandionetsa ine mbeu zako zomwe.
12 Ndipo Yosefe anaturutsa iwo pakati pa maondo ace, nawerama ndi nkhope yace pansi.
13 Ndipo Yosefe anatenga iwo onse awiri, Efraimu m'dzanja lace lamanja ku dzanja lamanzere la Yakobo, ndi Manase m'dzanja lace lamanzere ku dzanja lamanja la Israyeli, nadza nao pafupi ndi iye.
14 Ndipo Israyeli anatambalitsa dzanja lace lamanja, naliika pa mutu wa Efraimu, amene ndiye wamng'ono, ndi dzanja lace lamanzere pa mutu wa Manase anapingasitsa manja ace dala; cifukwa Manase anali woyamba.
15 Ndipo anadalitsa Yosefe, nati, Mulungu, pamaso pace anayenda makolo anga Abrahamu ndi Isake, Mulungu amene anandidyetsa ine nthawi zonse za moyo wanga kufikira lero,
16 mthenga amene anandiombola ine ku zoipa zonse, adalitse anyamatawa; dzina langa lichulidwe pa iwo, ndi dzina la makolo anga Abrahamu ndi Isake; iwo akule, nakhale khamu pakati pa dziko lapansi.
17 Ndipo pamene Yosefe anaona kuti atate wace anaika dzanja lace lamanja pa mutu wa Efraimu, kudamuipira iye; ndipo anatukula dzanja la atate wace, kulicotsa pa mutu wa Efraimu ndi kuliika pa muta wa Manase.
18 Ndipo Yosefe anati kwa atate wace, Msatero atate wanga, cifukwa uyu ndi woyamba; ikani dzanja lanu lamanja pa mutu wace.
19 Koma anakana atate wace, nati, Ndidziwa mwananga, ndidziwa; Iyenso adzakhala mtundu wa anthu, iyenso adzakula; koma mphwace adzakhala wamkuru ndi iye, ndipo mbeu zace zidzakhala mitundu yambirimbiri.
20 Ndipo anadalitsa iwo tsiku lomwelo, nati, Mwa iwe Israyeli adzadalitsa, kuti, Mulungu akuyese iwe monga Efraimu ndi monga Manase; ndipo anaika Efraimu woyamba wa Manase.
21 Ndipo Israyeli anati kwa Yosefe, Taona, ndirinkufa ine; Mulungu adzakhala ndi iwe, adzakubwezanso iwe ku dziko la makolo ako.
22 Ndipo ine ndakupatsa iwe gawo limodzi loposa la abale ako, limene ndinalanda m'dzanja la Aamori ndi lupanga langa ndi uta wanga.
1 Ndipo Yakobo anaitana ana ace amuna, nati, Sonkhanani inu, kuti ndikuuzeni inu cimene cidzakugwerani inu masiku akudzawo.
2 Sonkhanani, tamvani, ana amuna a Yakobo: Tamverani Israyeli atate wanu:
3 Rubeni, ndiwe woyamba wanga, mphamvu yanga ndi ciyambi ca mphamvu yanga; Ulemu wopambana, ndi mphamvu yopambana.
4 Wobwabwada ngati madzi; sudzapambana; Cifukwa unakwera pa kama wa atate wako; Pamenepo unaipitsapo; anakwera paja ndigonapo.
5 Simeoni ndi Levi ndiwo abale; Zida za mphulupulu ndizo malupanga ao.
6 Mtima wangawe, usalowe mu ciungwe cao; Ulemerero wanga, usadziphatike pa masonkhano ao; Cifukwa m'kukwiya kwao anapha munthu, M'kufuna kwao anapundula ng'ombe.
7 Kutembereredwekukwiyakwao, cifukwa kunali koopsya; Ndi kupsya mtima kwao, cifukwa kunali kwankharwe; Ndidzawagawanitsa m'Yakobo Ndidzabalalitsa iwo m'Israyeli.
8 Yuda, abale ako adzakuyamika iwe; Dzanja lako lidzakhala pa khosi la adani ako; Ana amuna a atate wako adzakuweramira.
9 Yuda ndi mwana wa mkango, Kucokera kuzomotola, mwananga, wakwera; Anawerama pansi, anabwatama ngati mkango, Ndipo ngati mkango waukazi; ndani adzamukitsa iye?
10 Ndodo yacifumu siidzacoka mwa Yuda, Kapena wolamulira pakati pa mapazi ace, Kufikira atadza Silo; Ndipo anthu adzamvera iye.
11 Adamanga mwana wa kavalo wace pampesa, Ndi mwana wa buru wace pa mpesa wosankhika; Natsuka malaya ace m'vinyo, Ndi copfunda cace m'mwazi wa mphesa.
12 Maso ace adzafiira ndi vinyo, Ndipo mana ace adzayera ndi mkaka.
13 Zebuloni adzakhala m'doko la kunyanja; Ndipo iye adzakhala doko la ngalawa; Ndipo malire ace adakhala pa Zidoni.
14 Isakara ndiye buru wolimba, Alinkugona pakati pa makola;
15 Ndipo anaona popumulapo kuti panali pabwino, Ndi dziko kuti linali lokondweretsa; Ndipo anaweramitsa phewa lace kuti anyamule, Nakhala kapolo wakugwira nchito ya msonkho,
16 Dani adzaweruza anthu ace, Monga limodzi la mafuko a Israyeli.
17 Dani adzakhala njoka m'khwalala, Songo panjira, Imene iluma zitende za kavalo, Kuti womkwera wace agwe cambuyo.
18 Ndadikira cipulumutso canu, Yehova.
19 Ndi Gadi, acifwamba adzampsinja iye; Koma iye adzapsinja pa citende cao.
20 Ndi Aseri, cakudya cace ndico mafuta, Ndipo adzapereka zolongosoka zacifumu.
21 Nafitali ndi nswala yomasuka; Apatsa mau abwino.
22 Yosefe ndi nthambi yobala, Nthambi yobala pambali pa kasupe; Nthambi zace ziyangayanga palinga.
23 Eni uta anabvutitsa iye kwambiri, Namponyera iye, namzunza:
24 Koma uta wace unakhala wamphamvu, Ndi mikono ya manja ace inalimbitsidwa Ndi manja a Wamphamvu wa Yakobo. (Kucokera kumeneko ndi mbusa, mwala wa Israyeli,)
25 Ndi Mulungu wa atate wako amene adzakuthangata iwe, Ndi Wamphamvuyonse, amene adzakudalitsa iwe Ndi madalitso a Kumwamba, Madalitso a madzi akuya akukhala pansi, Madalitso a mabere, ndi a mimba.
26 Madalitso a atate wako Apambana mphamvu ndi madalitso a makolo anga, Kufikira ku malekezero a patari a mapiri a cikhalire; Adzakhala pa mutu wa Yosefe, Ndi pakati pa mutu wa iye amene ali wolekanitsidwa ndi abale ace.
27 Benjamini ndiye mmbulu wakulusalusa; M'mamawa adzadya comotola, Madzulo adzagawa zofunkha.
28 Awa onse ndiwo mafuko khumi ndi awiri a Israyeli: izo ndizo zomwe ananena kwa iwo atate wao nawadalitsa; yense monga mdalitso wace anawadalitsa.
29 Ndipo analangiza iwo nati kwa iwo, Ine nditi ndisonkhanizidwe kwa anthu a mtundu wanga; mundiike ine pamodzi ndi makolo anga m'phanga liri m'munda wa Efroni Mhiti,
30 m'phanga liri m'munda wa Makipela, umene uli patsogolo pa Mamre, m'dziko la Kanani, limene Abrahamu analigula kwa Efroni Mhiti pamodzi ndi munda, likhale poikira pace:
31 pamenepo anaika Abrahamu ndi Sara mkazi wace; pamenepo anaika Isake ndi Rebeka mkazi wace: pamenepo ndinaika Leya:
32 munda ndi phanga liri m'menemo, zinagulidwa kwa ana a Heti.
33 Pamene Yakobo anatha kulangiza ana ace amuna, anafunya mapazi ace pakama, natsirizika, nasonkhanizidwa kwa anthu a mtundu wace.
1 Ndipo Yosefe anagwapa nkhope ya atate wace, namlirira iye nampsompsona iye.
2 Ndipo Yosefe anauza akapolo ace asing'anga kutiakonze atate wace: ndi mankhwala osungira thupi: ndipo asing'anga anakonza Israyeli.
3 Ndipo anatha masiku ace makumi anai a iye; cifukwa comweco amatsiriza masiku akukonza thupi; ndipo Aaigupto anamlira iye masiki makumi asanu ndi awiri.
4 Atapita masiku akumlira iye Yosefe anati kwa mbumba ya Farao kuti, Ngatitu ndapeza ufulu pamase panu, nenanitu m'makutu a Parae kuti,
5 Atate wanga anandilumbi ritsa ine, kuti, Taona, ndirinkufa m'manda m'mene ndadzikonzeran ndekha m'dziko la Kanani, m'menemo udzandiika ine. Tsopano mundi loletu, ndikwereko, ndipite, ndikaike atate wanga, nditatero ndidzabwe ranso.
6 Ndipo Farao anati, Pita kaike atate wako, monga iye anaku lumbiritsa iwe.
7 Ndipo Yosefe anapita kukaika atate wace; ndipo anakwera pamodzi ndi akapolo onse a Farao, ndi akuru a pa mbumba yace, ndi akuru onse a m'dziko la Aigupto,
8 ndi mbumba yonse ya Yosefe ndi abale ace, ndi mbumba ya atate wace: ang'ono ao okha, ndi nkhosa zao, ndi ng'ombe zao, anazisiya m'dziko la Goseni.
9 Ndipo anakwera pamodzi ndi iye magareta ndi apakavalo; ndipo panali khamc lalikuru.
10 Ndipo anafika pa dwale la Atadi, liri tsidya lija la Yordano, pamenepo anamlira maliro a atate wace masiku asanu ndi limodzi.
11 Ndipo pamene anthu okhala m'dzikomo; Akanani, anaona maliro a m'dwale la Atadi, anati, Awa ndi maliro akuru a Aaigupto: cifukwa cace dzina la pamenepo linachedwa Abeli-mizraimu, pali tsidya lija la Yordano.
12 Ndipo ana ace amuna anamcitira iye monga anawalamulira iwo;
13 cifukwa kuti ana ace amuna anamnyamula iye kulowa naye m'dziko la Kanani, ndi kumuika iye m'phanga la munda wa Makipela, limene Abrahamu analigula pamodzi ndi munda, likhale poikira pace, kwa Efroni Mhiti, patsogolo pa Mamre.
14 Ndipo ataika atate wace, Yosefe mabwera ku Aigupto, iye ndi abale ace, ndi onse amene anakwera pamodzi naye kukaika atate wace.
15 Ndipo pamene abale ace a Yosefe anaona kuti atate wao anafa, anati, Kapena Yosefe adzatida ife, ndipo adzatibwezera ife zoipa zonse tidamcitira iye.
16 Ndipo anatumiza mthenga kwa Yosefe kuti, Atate wathu asanafe analamulira, kuti,
17 Muziti cotero kwa Yosefe, Mukhululukiretu tsopano kulakwa kwa abale anu, ndi kucimwa kwao, cifukwa kuti anakucitirani inu coipa; tsopano mutikhululukiretu kulakwa kwa aka polo a Mulungu wa atate wanu. Ndipo Yosefe analira pamene iwo ananena ndi iye.
18 Ndiponso abale ace anamuka namgwadira pamaso pace; nati, Taonani, ife ndife akapolo anu.
19 Ndipo Yosefe anati kwa iwo, Musaope; pakuti ndiri ine kodi m'malo a Mulungu?
20 Koma inu, munandipangira ine coipa; koma Mulungu anacipangira cabwino, kuti kucitike monga lero, kupulumutsa amoyo anthu ambiri,
21 Ndipo tsopano musaope; Ine ndidzacereza inu, ndi ana anu ang'ono. Ndipo anawatonthoza iwo mitima yao, nanena nao mokoma mtima.
22 Ndipo Yosefe anakhala m'Aigupto, iye, ndi mbumba ya atate wace; ndipo Yosefe anakhala ndi movo zaka zana limodzi ndi khumi.
23 Ndipo Yosefe anaona ana a Efraimu a mbadwo wacitatu; ananso a Makiri mwana wamwamuna wa Manase anabadwa pa maondo a Yosefe.
24 Yosefe ndipo anati kwa abale ace, Ndirinkufa ine, koma Mulungu adzaonekera kwa inu, adzakucotsani inu m'dziko muno kubwera kunka ku dziko limene analumbirira kwa Abrahamu ndi kwa Isake, ndi kwa Yakobo
25 Ndipo Yosefe analumbiritsa ana a Israyeli kuti, Mulungu adzaonekera kwa inu ndithu, ndipo mudzakwera nao mafupa anga kucokera kuno.
26 Ndipo anafa Yosefe, anali wa zaka zana limodzi ndi khumi; ndipo anakonza thupi lace ndi mankhwala osungira, ndipo ariamuika iye m'bokosi m'Aigupto.