1

1 NDIPO mau a Yehova anadza kwa Yona mwana wa Amitai, ndi kuti,

2 Nyamuka, pita ku Nineve, mudzi waukuruwo, nulalikire motsutsana nao; pakuti coipa cao candikwerera pamaso panga.

3 Koma Yona ananyamuka kuti athawire ku Tarisi, kuzemba Yehova; ndipo anatsikira ku Yopa, napezako combo comuka ku Tarisi, napereka ndalama zace, natsikira m'menemo, kuti apite nao ku Tarisi kuzemba Yehova.

4 Koma Yehova anautsa cimphepo cacikuru panyanja, ndipo panali namondwe wamkuru panyanja, ndi combo cikadasweka.

5 Pamenepo amarinyero anacita mantha, napfuulira yense kwa mlungu wace, naponya m'nyanja akatundu anali m'combo kucipepuza. Koma Yona adatsikira m'munsi mwa combo, nagona tulo tofa nato.

6 Ndipo mwini combo anadza kwa iye, nanena naye, Utani iwe wam'tulo? uka, itana Mulungu wako, kapena Mulunguyo adzatikumbukila tingatayike.

7 Ndipo anati yense kwa mnzace, Tiyeni ticite maere, kuti tidziwe coipa ici catigwera cifukwa ca yani. M'mwemo anacita maere, ndipo maere anagwera Yona.

8 Pamenepo anati kwa iye, Utiuzetu coipa ici catigwera cifukwa ca yani? nchito yako njotani? ufuma kuti? dziko lako nliti? nanga mtundu wako?

9 Ndipo ananena nao, Ndine Mhebri, ndiopa Yehova Mulungu wa Kumwamba amene analenga nyanja ndi mtunda.

10 Pamenepo amunawo anaopa kwambiri, nati kwa iye, Ici nciani wacicita? Pakuti amunawo anadziwa kuti anathawa pamaso pa Yehova, popeza adawauza.

11 Tsono anati kwa iye, Ticitenji nawe, kuti nyanja iticitire bata? popeza namondwe anakula-kulabe panyanja.

12 Ndipo anati nao, Mundinyamule ndi kundiponya m'nyanja, momwemo nyanja idzacitira inu bata; pakuti ndidziwa kuti namondwe wamkuru amene wakugwerani cifukwa ca ine.

13 Koma amunawo anapalasa kubwerera kumtunda, koma sanathe; pakuti namondwe wa panyanja anakulakula mokomana nao.

14 Pamenepo anapfuulira kwa Yehova, nati, Tikupemphanitu, Yehova, tisatayike cifukwa ca moyo wa munthu uyu, musatisenzetse mwazi wosacimwa; pakuti, Inu Yehova, mwacita monga mudakomera Inu.

15 Momwemo ananyamula Yona, namponya m'nyanja; ndipo nyanja inaleka kukokoma kwace.

16 Ndipo amunawo anaopa Yehova ndi manthaakuru, namphera Yehova nsembe, nawinda.

17 Koma Yehova anaikiratu cinsomba cacikuru cimeze Yona; ndipo Yona anali m'miroba mwa nsombayi masiku atatu usana ndi usiku.

2

1 Pamenepo Yona anapemphera kwa Yehova Mulungu wace ali m'mimba mwa nsombayo.

2 Ndipo anati, Ndinaitana Yehova m'nsautso yanga, Ndipo anandiyankha ine; Ndinapfuula ndiri m'mimba ya manda, Ndipo munamva mau anga.

3 Pakuti munandiponya mwakuya m'kati mwa nyanja, Ndipo madzi anandizinga; Mapfunde anu onse a nyondonyondo anandimiza.

4 Ndipo ndinati, Ndatayika ndicoke pamaso panu; Koma ndidzapenyanso Kacisi wanu wopatulika.

5 Madzi anandizinga mpaka moyo wanga, Madzi akuya anandizungulira, Kayandeyande wa m'nyanja anandikulunga mutu.

6 Ndinatsikira ku matsinde a mapiri, Mipingiridzo ya dziko inanditsekereza kosatha; Koma munandikwezera moyo wanga kuucotsa kucionongeko, Yehova Mulungu wanga.

7 Pokomoka moyo wanga m'kati mwanga ndinakumbukila Yehova; Ndi pemphero langa linafikira Inu m'Kacisi wanu wopatulika.

8 Iwo osamalira mabodza opanda pace Ataya cifundo cao cao.

9 Koma ine ndidzakupherani Inu nsembe ndi mau akuyamika, Ndidzakwaniritsacowindacanga. Cipulumutso nca Yehova.

10 Pamenepo Yehova analankhula ndi nsombayo, ndipo inamsanzira Yona kumtunda.

3

1 Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yona nthawi yaciwiri, ndi kuti,

2 Nyamuka, pita ku Nineve mudzi waukuru uja, nuulalikire uthenga umene ndikuuza.

3 Ndipo Yona ananyamuka, napita ku Nineve, monga mwa mau a Yehova. Koma Nineve ndiwo mudzi waukuru pamaso pa Yehova, wa ulendo wa masiku atatu.

4 Ndipo Yona anayamba kulowa mudziwo ulendo wa tsiku limodzi, nalalikira, nati, Atsala masiku makumi anai ndipo Nineve adzapasuka.

5 Ndipo anthu a Nineve anakhulupirira Mulungu, nalalikira cosala, nabvala ciguduli, kuyambira wamkuru kufikira wamng'ono wa iwowa.

6 Pakuti mau awa anafikira mfumu ya Nineve, ndipo Inanyamuka ku mpando wace wacifumu, nibvula copfunda cace, nipfunda ciguduli, nikhala m'mapulusa.

7 Ndipo analalikira, nanena m'Nineve mwa lamulo la mfumu ndi nduna zace, ndi kuti, Ngakhale munthu kapena nyama, ngakhale ng'ombe kapena nkhosa, zisalawe kanthu, zisadye, zisamwe madzi;

8 koma zipfundidwe ndi ciguduli munthu ndi nyama, nizipfuulire kolimba kwa Mulungu; ndipo abwere yense kuleka njira yace yoipa, ndi ciwawa ciri m'manja mwace.

9 Kaya, akatembenuka Mulungu, ndi kuleka kubwera ku mkwiyo wace waukali, kuti tisatayike,

10 Ndipo Mulungu anaona nchito zao, kuti anabwera kuleka njira yao yoipa; ndipo Mulungu analeka coipa adanenaci kuti adzawacitira, osacicita.

4

1 Koma sikudakomera Yona konse, ndipo anapsa mtima.

2 Ndipo anapemphera kwa Yehova, nati, Ha, Yehova! si ndiwo mau anga ndikali m'dziko langa? cifukwa cace ndinafulumira kuthawira ku Tarisi, pakuti ndinadziwa kuti Inu ndinu Mulungu wacisomo ndi wodzala cifundo, wolekerera ndi wokoma mtima mocuruka, ndi woleka coipaco.

3 Ndipo tsopano, Yehova, mundicotseretu moyo wanga, kundikomera ine kufa, osakhala ndi moyo ai.

4 Ndipo Yehova anati, Uyenera kupsa mtima kodi?

5 Pamenepo Yona anaturuka m'mudzi, nakhala pansi kum'mawa kwa mudzi, nadzimangira komweko thandala, nakhala pansi pace mumthunzi mpaka adzaona cocitikira mudzi.

6 Ndipo Yehova Mulungu anaikiratu msatsi, naumeretsera Yona, ucite mthunzi pamutu pace, kumlanditsa m'nsautso yace. Ndipo Yona anakondwera kwambiri cifukwa ca msatsiwo.

7 Koma Mulungu anauikira mphanzi pakuca m'mawa mwace, ndiyo inadya msatsi, nufota.

8 Ndipo kunali, poturuka dzuwa Mulungu anaika mphepo ya kum'mawa yotentha, ndipo dzuwa linatentha mutu wace wa Yona, nalefuka iye, nadzipempherera kuti afe; nati, Kundikomera ine kufa, kukhala ndi moyo ai.

9 Ndipo Mulungu anati kwa Yona, Uyenera kodi kupsa mtima cifukwa ca msatsiwo? Nati iye, Ee, kundiyenera ine kupsa mtima mpaka imfa.

10 Ndipo Yehova anati, Unacitira cifundo msatsiwo umene sunagwirapo nchito, kapena kuumeretsa, umene unamera usiku, nutha usiku;

11 ndipo sindiyenera Ine kodi kucitira cifundo Nineve mudzi waukuru uwu; m'mene muli anthu oposa zikwi zana limodzi mphambu zikwi makumi awiri osadziwa kusiyanitsa pakati pa dzanja lao lamanja ndi lamanzere, ndi zoweta zambiri zomwe?