1 CIYAMBI cace ca Uthenga Wabwino wa Yesu Kristu, Mwana wa Mulungu.
2 Monga mwalembedwa m'Yesaya mneneri, Ona, ndituma mthenga wanga patsogolo pa nkhope yanu, Amene adzakonza njira yanu;
3 Mau a wopfuula m'cipululu, Konzani khwalala la Ambuye, Lungamitsani njira zace;
4 Yohane anadza nabatiza m'cipululu, nalalikira ubatizo wa kutembenuka mtima wakuloza ku cikhululukiro ca macimo.
5 Ndipo anaturuka a ku dziko lonse la Yudeya, ndi a ku Yerusalemu onse; nadza kwa iye nabatizidwa ndi iye mumtsinje Yordano, poulula macimo ao.
6 Ndipo Yohane anabvala ubweya wa ngamila, ndi lamba lacikopa m'cuuno mwace, nadya dzombe ndi uci wa kuthengo.
7 Ndipo analalikira, kuti, Wondipambana ine mphamvu akudza pambuyo panga, sindiyenera kuwerama kumasula lamba la nsapato zace ine.
8 Ndakubatizani inu ndi madzi; koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.
9 Ndipo kunali masiku omwewo, Yesu anadza kucokera ku Nazarete wa ku Galileya, nabatizidwa ndi Yohane m'Yordano.
10 Ndipo pomwepo, alimkukwera poturuka m'madzi, anaona Iye thambo litang'ambika, ndi Mzimu alikutsikira pa Iye monga nkhunda:
11 ndipo mau anaturuka m'thambo, Mwana wanga wokondedwa ndiwe, mwa Iwe ndikondwera bwino.
12 Ndipo pomwepo Mzimu anamkangamiza kunka kucipululu.
13 Ndipo anakhala m'cipululu masiku makumi anai woyesedwa ndi Satana; nakhala ndi zirombo, ndipo angelo anamtumikira.
14 Ndipo ataperekedwa Yohane, Yesu anadza ku Galileya, nalalikira uthenga wabwino wa Mulungu,
15 nanena, Nthawi yakwanira, ndipo Ufumu wa Mulungu wayandikira; tembenukani mtima, khulupirirani uthenga wabwino.
16 Ndipo pakuyenda m'mbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi Andreya, mbale wace wa Simoni, alinkuponya psasa m'nyanja; pakuti anali asodzi.
17 Ndipo Yesu ananena nao, Idzani pambuyo panga, ndipo ndidzakusandutsani inu asodzi a anthu.
18 Ndipo pomwepo anasiya makoka ao, namtsata Iye.
19 Ndipo atapita patsogolo pang'ono, anaona Yakobo, mwana wa Zebedayo, ndi Yohane mbale wace, iwonso anali m'combo nakonza makoka ao.
20 Ndipo pomwepo anawaitana: ndipo anasiya atate wao Zebedayo m'combomo pamodzi ndi anchito olembedwa, namtsata.
21 Ndipo iwo analowa m'Kapemao; ndipo pomwepo pa dzuwa la Sabata iye analowa m'sunagoge naphunzitsa,
22 Ndipo anazizwa ndi ciphunzitso cace; pakuti anaphunzitsa monga mwini mphamvu, si monga alembi.
23 Ndipo pomwepo panali munthu m'sunagoge mwao ali ndi mzimu wonyansa; ndipo anapfuula iye
24 kuti, Tiri ndi ciani ife ndi Inu Yesu wa ku Nazarete? Kodi mwadza kudzationonga ife? Ndikudziwani, ndinu Woyerayo wa Mulungu.
25 Ndipo Yesu anaudzudzula, kuti, Khala uli cete, nuturuke mwa iye.
26 Ndipo mzimu wonyansa, pomng'amba, ndi kupfuula ndi mau akuru, unaturuka mwa iye.
27 Ndipo anazizwa onse, kotero kuti anafunsana mwa iwo okha, kuti, Ici nciani? ciphunzitso catsopano! ndi mphamvu alamula ingakhale mizimu yonyansa, ndipo imvera Iye.
28 Ndipo mbiri yace inabuka pompaja ku dziko lonse la Galileya lozungulirapo.
29 Ndipo pomwepo, poturuka m'sunagoge, iwo analowa m'nyumba ya Simoni ndi Andreya pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane,
30 Ndipo mpongozi wace wa Simoni anali gone wodwala malungo; ndipo pomwepo anamuuza za iye:
31 ndipo anadza namgwira dzanja, namuutsa; ndipo malungo anamleka, ndipo anawatumikira iwo.
32 Ndipo madzulo, litalowa dzuwa, anadza nao kwa Iye onse akudwala, ndi akugwidwa ndi ziwanda.
33 Ndipo mudzi wonse unasonkhana pakhomo.
34 Ndipo anaciritsa anthu ambiri akudwala nthenda za mitundu mitundu, naturutsa ziwanda zambiri; ndipo sanalola ziwandazo zilankhule, cifukwa zinamdziwa Iye.
35 Ndipo m'mawa mwace anauka usikusiku, naturuka namuka kucipululu, napemphera kumeneko.
36 Ndipo Simoni ndi anzace anali naye anamtsata,
37 nampeza, nanena naye, Akufunani inu anthu onse.
38 Ndipo ananena nao, Tiyeni kwina, ku midzi iri pafupi apa, kuti ndilalikire komwekonso; pakuti ndadzera nchito imene.
39 Ndipo analowa m'masunagoge mwao m'Galileya monse, nalalikira, naturutsa ziwanda.
40 Ndipo anadza kwa Iye wodwala khate, nampempha Iye, namgwadira, ndi kunena ndi Iye, Ngati mufuna mukhoza kundikonza.
41 Ndipo Yesu anagwidwa cifundo, natansa dzanja namkhudza iye, nanena naye, Ndifuna; khala wokonzedwa.
42 Ndipo pomwepo khate linamcoka, ndipo anakonzedwa.
43 Ndipo anamuuzitsa, namturutsa pomwepo,
44 nanena naye, Ona, usati unene kanthu kwa munthu ali yense: koma muka, ukadzionetse kwa wansembe, nupereke pa makonzedwe ako 1 zimene adalamulira Mose, zikhale mboni kwa iwo.
45 Koma 2 iye anaturuka nayamba kulalikira ndithu, ndi kubukitsa mauwo, kotero kuti Yesu sanadziwa kulowansopoyera m'mudzi, koma anakhala padera m'mapululu; ndipo anadza kwa Iye anthu a ku malo onse.
1 Ndipo polowanso Iye m'Kapernao atapita masiku ena, kunamveka kuti ali m'nyumba.
2 Ndipo ambiri anaunjikana, kotero kuti anasowa malo, ngakhale pakhomo pomwe; ndipo analankhula nao mau.
3 Ndipo anadza kwa Iye otenga munthu wodwala manjenje, wonyamulidwa ndi anthu anai.
4 Ndipo pamene sanakhoza kufika kuli Iye, cifukwa ca khamu la anthu, anasasula chindwi pokhala Iye; ndipo pamene anatha kuliboola, anatsitsa mphasa m'mene alinkugonamo wodwala manjenjeyo,
5 Ndipo Yesu pakuona cikhulupiriro cao ananena ndi wodwala manjenje, Mwana, macimo ako akhululukidwa.
6 Koma anakhalapo ena a alembi akuganizira mumtima mwao,
7 Munthu amene atero bwanji? acita mwano; akhoza ndani kukhululukira macimo, koma mmodzi, ndiye Mulungu?
8 Ndipo pomwepo Yesu pozindikira mumtima mwace kuti alikuganizira comweco mwa iwo okha, ananena nao, Muganiza bwanji zinthu izi m'mitima yanu?
9 Capafupi nciti, kapena kuuza wodwala manjenje kuti, Macimo ako akhululukidwa; kapena kuti, Nyamuka, senza mphasa yako, nuyende?
10 Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa munthu ali mwini ulamuliro wakukhululukira macimo pa dziko lapansi (ananena ndi wodwala manjenje),
11 Ndikuuza iwe, Nyamuka, senza mphasa yako, numuke kwanu.
12 Ndipo ananyamuka iye pomwepo, nasenza mphasa, naturuka pamaso pa iwo onse; kotero kuti anadabwa onse, nalemekeza Mulungu, nanena kuti, Zotere sitinaziona ndi kale lonse.
13 Ndipo anaturukanso kunka m'mbali mwa nyanja; ndipo linadza kwa Iye khamu lonse la anthu, ndipo anawaphunzitsa.
14 Ndipo pakumuka, anaona Levi mwana wa Alifeyu alikukhala polandira msonkho, ndipo ananena naye, Tsata Ine.
15 Ndipo ananyamuka namtsata Iye. Ndipo kunali kuti anakhala pakudya m'nyumba mwace, ndipo amisonkho ndi ocimwa ambiri anakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ace, pakuti anali ambiri, ndipo anamtsata Iye.
16 Ndipo alembi a kwa Afarisi, pakuona kuti alinkudya nao ocimwa ndi amisonkho, ananena ndi ophunzira ace, Uyu akudya ndi kumwa nao amisonkho ndi ocimwa.
17 Ndipo pamene Yesu anamva ici, ananena nao, Akulimba safuna sing'anga, koma odwala ndiwo; sindinadza kudzaitana olungama, koma ocimwa.
18 Ndipo ophunzira a Yohane ndi Afarisi analinkusala kudya; ndipo anadza, nanena ndi Iye, Bwanji asala kudya ophunzira a Yohane, ndi ophunzira a Afarisi, koma ophunzira anu sasala kudya?
19 Ndipo Yesu ananena nao, Kodi akhoza kusala kudya anyamata a ukwati pamene mkwati ali pamodzi nao? pokhala ali naye mkwati pamodzi ndi iwo sakhoza kusala.
20 Koma adzadza masiku, pamene mkwati adzacotsedwa kwa iwo, ndipo pamenepo adzasala kudya tsiku lomwelo.
21 Palibe munthu asokerera cigamba ca nsaru yaiwisi pa copfunda cakale; pena cimene coti cidzakonza cizomolapo, catsopanoco cizomoka pa cakaleco, ndipo ciboo cikulapo.
22 Ndipo palibe munthu amatsanulira vinyo watsopano m'matumba akale: pena vinyo adzaphulitsa matumba, ndipo aonongeka vinyo, ndi matumba omwe: koma vinyo watsopano amatsanulira m'matumba atsopano.
23 Ndipo kunali kuti anapita Iye pakati pa minda dzuwa la Sabata; ndipo ophunzira ace poyenda anayamba kubudula ngala za dzinthu.
24 Ndipo Afarisi ananena ndi Iye, Taona, acitiranji cosaloleka kucitika dzuwa la Sabata?
25 Ndipo ananena nao, Simunawerenga konse cimene anacicita Davide, pamene adasowa, namva njala, iye ndi iwo amene anali pamodzi naye?
26 Kuti, analowa m'nyumba ya Mulungu masiku a Abyatara, mkulu wa ansembe, ndipo anadya mikate yoonetsera, yosaloleka kudya ena, koma ansembe okha, ndipo anawapatsanso iwo amene anali naye?
27 Ndipo ananena nao, Sabata linaikidwa cifukwa ca munthu, si munthu cifukwa ca Sabata;
28 motero Mwana wa munthu ali mwini dzuwa la Sabata lomwe.
1 Ndipo analowanso m'sunagoge; ndipo munali munthu m'menemo ali ndi dzanja lace lopuwala.
2 Ndipo anamuyang'anira Iye, ngati adzamciritsa dzuwa la Sabata; kuti ammange mlandu.
3 Ndipo ananena ndi munthu ali ndi dzanja lopuwala, Taimirira pakati.
4 Ndipo ananena kwa iwo, Kodi nkuloledwa dzuwa la Sabata kucita zabwino, kapena zoipa? kupulumutsa moyo kapena kupha? Koma anakhala cete.
5 Ndipo m'mene anawaunguza ndi mkwiyo, ndi kumva cisoni cifukwa ca kuuma kwa mitima yao, ananena kwa munthuyo, Tambasula dzanja lako. Ndipo analitambasula; ndipo linacira dzanja lace.
6 Ndipo Afarisi anaturuka, ndipo pomwepo anamkhalira upo ndi Aherode, wakumuononga Iye.
7 Ndipo Yesu anacokako pamodzi ndi ophunzira ace nanka kunyanja: ndipo linamtsata khamu lalikuru la a ku Galileya, ndi aku Yudeya,
8 ndi a ku Yerusalemu, ndi a ku Idumeya, ndi a ku tsidya lina la Y ordano, ndi a kufupi ku Turo ndi Sidoni, khamu lalikuru, pakumva zazikuruzo anazicita, linadza kwa Iye.
9 Ndipo anati kwa ophunzira ace, kuti kangalawa kamlinde Iye, cifukwa ca khamulo, kuti angamkanikize Iye,
10 pakuti adawaciritsa ambiri; kotero kuti onse akukhala nazo zowawa anakanikiza Iye, kuti akamkhudze.
11 Ndipo mizimu yonyansa, m'mene inamuona Iye, inamgwadira, nipfuula, niti, Inu ndinu Mwana wa Mulungu.
12 Ndipo anailimbitsira mau kuti isamuulule Iye.
13 Ndipo anakwera m'phiri, nadziitanira iwo amene anawafuna Iye mwini; ndipo anadza kwa Iye.
14 Ndipo anaika khumi ndi awiri, kuti akhale ndi Iye, ndi kuti akawatume kulalikira,
15 ndi kuti akhale nao ulamuliro wakuturutsa ziwanda.
16 Ndipo Simoni anamucha Petro;
17 ndi Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi Yohane mbale wace wa Yakobo, iwo anawacha Boanerge, ndiko kuti, Ana a bingu;
18 ndi Andreya, ndi Filipo, ndi Bartolomeyo, ndi Mateyu, ndi Tomasi, ndi Yakobo mwana wa Alifeyo, ndi Tadeyo, ndi Simoni Mkanani,
19 ndi Yudase Isikariote, ndiye amene anampereka Iye. Ndipo analowa m'nyumba.
20 Ndipo anthu ambiri anasonkhananso, kotero kuti sanathe iwo konse kudya.
21 Ndipo pamene abale ace anamva, anadza kudzamgwira Iye; pakuti anati adayaruka.
22 Ndipo alembi amene adatsika ku Yerusalemu ananena kuti, Ali naye Beelzibule, ndipo, Ndi mkuru wao wa ziwanda aturutsa ziwanda.
23 Ndipo m'mene adawaitana iwo, ananena nao m'mafanizo, Satana angathe bwanji kuturutsa Satana?
24 Ndipo ufumu ukagawanika pa uwu wokha, sukhoza kukhazikika.
25 Ndipo nyumba ikagawanika pa iyo yokha, siikhoza kukhazikika nyumbayo,
26 Ndipo Satana akadziukira mwini yekha, nagawanika, sakhoza kukhazikika, koma atsirizika.
27 Komatu palibe munthu akhoza kulowa m'nvumba ya mwini mphamvu, ndi kufunkha akatundu ace, koma athange wamanga mwini mphamvuyo; ndipo pamenepo adzafunkha za m'nyumba mwace.
28 Indetu, ndinena ndi inu, Adzakhululukidwa macimo onse a ana a anthu, ndi zamwano ziri zonse adzacita mwano nazo;
29 koma ali yense adzacitira Mzimu Woyera mwano alibe kukhululukidwa nthawi yonse, koma anaparamuladi cimo losatha;
30 pakuti adanena, Ali ndi mzimu wonyansa.
31 Ndipo anadza amace ndi abale ace; naima kunja, namtumira uthenga kumuitana.
32 Ndipo anthu ambiri anakhala pansi pomzinga; nanena kwa Iye, Onani, amanu ndi abale anu ali kunja akufunani Inu.
33 Ndipo anawayankha nanena, Amai wanga ndi abale anga ndani?
34 Ndipo anawaunguza-unguza iwo akumzingawo, nanena, Taonani, amai wanga ndi abale anga.
35 Pakuti ali yense acita cifuniro ca Mulungu, yemweyo ndiye mbale wanga, ndi mlongo, ndi amai.
1 Ndipo anayambanso kuphunzitsa pambali pa nyanja, Ndipo anasonkhana kwa Iye khamu lalikurukuru, kotero kuti analowa Iye mungalawa, nakhala m'nyanja; ndipo khamu lonse linakhala pamtunda m'mbali mwa nyanja.
2 Ndipo anawaphunzitsa zinthu zambiri m'mafanizo, nanena nao m'ciphunzitso cace,
3 Mverani: taonani, wofesa anaturuka kukafesa;
4 ndipo kunali, m'kufesa kwace, zina zinagwa m'mbali mwanjira, ndi mbalamezinadza ndi kuzitha kudya,
5 Ndipo zina zinagwa pa nthaka yathanthwe, pamene panalibe nthaka yambiri; ndipo pomwepo zinamera, cifukwa zinalibe nthaka yakuya;
6 ndipo litakwera dzuwa zinapserera; ndipo popeza zinalibe mizu zinakhwinyata.
7 Ndipo zina zinagwa paminga, ndipominga inakula, nizitsamwitsa, ndipo sizinabala zipatso.
8 Ndipo zina zinagwa m'nthaka yabwino, ndipo zinapatsa zipatso, ndi kukula ndi kucuruka; ndipo zinabala kupindula makumi atatu, ndi makumi asanundi limodzi, ndi makumi khumi.
9 Ndipo ananena, Amene ali nao makutu akumva amve.
10 Ndipo pamene anakhala pa yekha, iwo amene anali pafupi ndi Iye pamodzi ndi khumi ndi awiriwo anamfunsa za mafanizo.
11 Ndipo Iye ananena nao, Kwa inu kwapatsidwa cinsinsi ca Ufumu wa Mulungu; koma kwa iwo ali kunja zonse zicitidwa m'mafanizo;
12 kuti kupenya apenye, koma asazindikire; ndipo kumva amve, koma asadziwitse; kuti pena angatembenuke, ndi kukhululukidwa.
13 Ndipo ananena nao, Simudziwa kodi fanizo ili? mukazindikira bwanji mafanizo onse?
14 Wofesa afesa mau.
15 Ndipo iwo ndiwo a m'mbali mwa njira mofesedwamo mau; ndipo pamene anamva, pomwepo akudza Satana nacotsa mau ofesedwa mwa iwo.
16 Ndipo momwemonso iwo ndiwo amene afesedwa pathanthwe, atamva mau, awalandira pomwepo ndi kusekera;
17 ndipo alibe mizu mwa iwo okha, koma akhala kanthawi; pamenepo pakudza masautso kapena mazunzo cifukwa ca mau, pomwepo akhumudwa.
18 Ndipo ena ndiwo akufesedwa kuminga; iwo ndiwo amene adamva mau,
19 ndipo malabadiro a dziko lapansi, ndi cinyengo ca cuma, ndi kulakalaka kwa zinthu zina, zilowamo, zitsamwitsa mau, ndipo akhala opanda cipatso.
20 Ndipo iwo ofesedwa pa nthaka yabwino ndiwo oterewa akumva mau, nawalandira, nabala zipatso zakupindula makumi atatu, ndi makumi asanu ndi limodzi, ndi makumi khumi.
21 Ndipo ananena ndi iwo, Kodi atenga nyali kuti akaibvundikire mbiya, kapena akaiike pansi pa kama, osati kuti akaiike pa coikapo cace?
22 Pakuti kulibe kanthu kobisika, koma kuti kaonetsedwe; kapena kulibe kanthu kanakhala kam'tseri, koma kuti kakaululidwe.
23 Ngati munthu ali nao makutu akumva, amve.
24 Ndipo ananena nao, Yang'anirani cimene mukumva; ndi muyeso umene muyesera nao udzayesedwa kwa inu; ndipo kudzaonjezedwa kwa inu.
25 Pakuti kwa iye amene ali nako kanthu, kadzapatsidwa; ndipo kwa iye amene alibe kanthu, kadzacotsedwa ngakhale kanthu kali konse ali nako.
26 Ndipo ananena, Ufumu wa Mulungu uli wotero, monga ngati munthu akataya mbeu panthaka;
27 nakagona ndi kuuka, usiku ndi usana, ndipo mbeu zikamera, ndi kukula, iye sadziwa umo zicitira.
28 Nthaka ibala zipatso zace yokha; uyamba mmera, zitsata ngala, pamenepo maso okhwima m'ngalamo.
29 Pakucha zipatso, pamenepo atumiza zenga, pakuti nthawi yakumweta yafika.
30 Ndipo ananena, Tidzafaniziranji Ufumu wa Mulungu? kapena tidzaulinganiza ndi fanizo lotani?
31 Ngati mbeu yampiru, imene ikafesedwapanthaka, ingakhale icepa ndi mbeu zonse za padziko,
32 koma pamene ifesedwa, imera nikula koposa zitsamba zonse, nicita nthambi zazikuru; kotero kuti mbalame za m'mlengalenga zikhoza kubindikira mumthunzi mwace.
33 Ndipo ndi mafanizo otere ambiri analankhula nao mau, 1 monga anakhoza kumva;
34 ndipo sanalankhula nao wopanda fanizo: koma m'tseri anatanthauzira zonse kwa ophunzira ace.
35 Ndipo dzuwa lomwelo, pofika madzulo, ananena kwa iwo, Tiolokere tsidya lina.
36 Ndipo posiya khamulo anamtenga apite nao, monga momwe anali, mungalawa. Ndipo panali ngalawa zina pamodzi ndi Iye.
37 Ndipo panauka namondwe wamkuru wa mphepo, ndi mafunde angabvira mungalawa, motero kuti ngalawa inayamba kudzala.
38 Ndipo Iye mwini anali kutsigiro, nagona tulo pamtsamiro; ndipo anamuutsa Iye nanena kwa Iye, Mphunzitsi, kodi simusamala kuti titayika ife?
39 Ndipo anauka, nadzudzula mphepo, nati kwa nyanja, kuti, Tonthola, khala bata. Ndipo mphepo inaleka, ndipokunagwa bata lalikuru.
40 Ndipo ananena nao, Mucitiranji mantha? kufikira tsopano mulibe cikhulupiriro kodi?
41 Ndipo iwo anacita mantha akuru, nanenana wina ndi mnzace, Uyu ndani nanga, kuti ingakhale mphepo ndi nyanja zimvera Iye?
1 Ndipo anafika tsidya lina la nyanja, ku dziko la Agerasa,
2 Ndipo pameneadaturuka mungalawa, pomwepo anakomana naye munthu woturuka kumanda wa mzimu wonyansa,
3 amene anayesa nyumba yace kumanda; ndipo palibe munthu anakhoza kummanganso, inde ngakhale ndi unyolo;
4 pakuti adafomangidwa kawiri kawiri ndi matangadza ndimaunyolo, ndipo anamwetula maunyolo, naduladula matangadza; ndipo palibe munthu anali ndi mphamvu yakumfuya.
5 Ndipo masiku onse, usiku ndi usana, anakhala m'manda ndi m'mapiri, napfuula, nadzitematema ndi miyala.
6 Ndipo pakuona Yesu kutali, anathamanga, namgwadira Iye;
7 ndipo anapfuula ndi mau olimba, nanena, Ndiri ndi ciani ine ndi Inu, Yesu Mwana wa Mulungu Wamkurukuru? Ndikulumbirirani pa Mulungu, msandizunze.
8 Pakuti ananena kwa iye, Turuka iwe, mzimu wonyansa, kwa munthuyu.
9 Ndipo anamfunsa, Dzina lako ndani? Ndipo ananena kwa Iye, Dzina langa ndine Legio; cifukwa tiri ambiri.
10 Ndipo anampempha Iye kwambiri kuti asaiturutsire kunja kwace kwa dziko.
11 Ndipo panali pamenepo gulu lalikuru la nkhumba zirinkudya kuphiri.
12 Ndipo inampempha Iye, kuti, Titumizeni ife mu nkhumbazo, kuti tilowe mu izo.
13 Ndipo anailolao Ndipo mizimu yonyansa inaturuka, nilowa mu nkhumba; ndipo gulu linatsika liwiro potsetsereka ndi kulowa m'nyanja, ndizo ngati zikwi ziwiri; ndipo zinatsamwa m'nyanja.
14 Ndipo akuziweta anathawa, nauza m'mudzi, ndi kwninda. Ndipo anadza kudzaona cocitikaco.
15 Ndipo anadza kwa Yesu, napenya wogwidwa ziwandayo alikukhala pansi, wobvala ndi wa nzeru zace zabwino, ndiye amene anali ndi legio; ndipo anaopa iwo.
16 Ndipo adapenyawo adawafotokozera umo anacitira ndi wogwidwa ziwandayo, ndi za nkhumbazo.
17 Ndipo anayamba kumpempha Iye kuti acoke m'malire ao,
18 Ndipo m'mene Iye analikulowa mungalawa, anampempha waziwanda uja kuti akhale ndi Iye.
19 Ndipo sanamlola, koma ananena naye, Muka kwanu kwa abale ako, nuwauze zinthu zazikuru anakucitira Ambuye, ndi kuti anakucitira cifundo.
20 Ndipo anamuka nayamba kulalikira ku Dekapoli zinthu zazikuru Yesu adamcitira iye; ndipo anthu onse anazizwa.
21 Ndipo pamene Yesu anaolokanso mungalawa tsidya lina, khamu lalikuru linasonkhana kwa Iye; ndipo Iye anali pambali pa nyanja.
22 Ndipo anadzako mmodzi wa akuru a sunagoge, dzina lace Yairo; ndipo pakuona Iye, anagwada pa mapazi ace, nampempha kwambiri,
23 nanena, kuti, Kamwana kanga kabuthu kalimkutsirizika; ndikupemphani Inu mufikeko, muike manja anu pa iko, kuti kapulwnuke, ndi kukhala ndi moyo.
24 Ndipo ananka naye pamodzi; ndipo khamu lalikuru linamtsata Iye, ndi kumkanikiza Iye.
25 Ndipo munthu wamkazi amene anali ndi nthenda yacidwalire zaka khwni ndi ziwiri,
26 ndipo anamva zowawa zambiri ndi asing'anga ambiri, nalipira zonse anali nazo osacira pang'ono ponse, koma makamaka nthenda yace idakula,
27 m'mene iye anamva mbiri yace ya Yesu, anadza m'khamu kumbuyo kwace, nakhudza cobvala cace.
28 Pakuti ananena iye, Ngati ndikakhudza ngakhale zobvala zace ndidzapulumutsidwa.
29 Ndipo pomwepo kasupe wa nthenda yace adaphwa; ndipo anazindikira m'thupi kuti anaciritsidwa cibvutiko cace.
30 Ndipo pomwepo Yesu, pamene anazindikira mwa Iye yekha kuti mphamvu idaturuka mwa Iye, anapotoloka m'khamu, nanena, Ndani anakhudza zobvala zanga?
31 Ndipo ophunzira ace ananena kwa Iye, Muona kuti khamu lirikukanikiza Inu, ndipo munena kodi, Wandikhudza ndani?
32 Ndipo Iye anaunguza-unguza kumuona iye amene adacita ici,
33 Koma mkaziyo anacita mantha, ndi kunthunthumira, podziwa cimene anamcitira iye, nadza, namgwadira, namuuza coona conse.
34 Ndipo anati kwa iye, Mwana wamkaziwe, cikhulupiriro, cako cakupulumutsa; muka mumtendere, nukhale wocira cibvutiko cako.
35 M'mene iye ali cilankhulire, anafika a ku nyumba ya mkuru wa sunagoge, nanena, kuti, Mwana wako wafa; ubvutiranjinso Mphunzitsi?
36 Koma Yesu wosasamala mau olankhulidwawo, ananena kwa mkuru wa sunagoge, Usaope, khulupirira kokha.
37 Ndipo sanalola munthu yense kutsagana naye, koma Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane mbale wace wa Yakobo.
38 Ndipo anafika ku nyumba kwace kwa mkuru wa sunagoge; ndipo anaona cipiringu, ndi ocita maliro, ndi akukuwa ambiri
39 Ndipo m'mene atalowa, ananena nao, Mubuma ndi kulira bwanji? Mwana sanafa, koma ali m'tulo.
40 Ndipo anamseka Iye pwepwete, Koma Iye anawaturutsa onse, natenga atate wa mwana, ndi amace, ndi ajawo anali naye, nalowa m'mene munali mwanayo.
41 Ndipo anagwira dzanja lace la mwana, nanena kwa iye, Talita koumi; ndiko kunena posandulika, Buthu, ndinena ndi iwe, Uka.
42 Ndipo pomwepo buthulo linauka, niliyenda; pakuti linali la zaka khumi ndi ziwiri. Ndipo anadabwa pomwepo ndi kudabwa kwakukuru.
43 Ndipo anawalamulira kwambiri kuti asadziwe ici munthu mmodzi, nawauza kuti ampatse iye kudya.
1 Ndipo Iye anaturuka kumeneko; nafika ku dziko la kwao; ndipo ophunzira ace anamtsata.
2 Ndipo pofika dzuwa la Sabata, anayamba kuphunzitsa m'sunagoge; ndipo ambiri anamva Iye, nazizwa, nanena, Uyu adazitenga kuti izi? Nzeru yopatsidwa kwa munthuyu njotani, ndi zamphamvu zotere zocitidwa ndi manja ace?
3 Si mmisiri wa mitengo uyu, mwana wa Mariya, mbale wao wa Yakobo, ndi Yose, ndi Yuda, ndi Simoni? Ndipo alongo ace sali nafe pano kodi? Ndipo anakhumudwa ndi Iye.
4 Ndipo Yesu ananena kwa iwo, Mneneri sakhala wopanda ulemu, koma m'dziko la kwao ndimo, ndi pakati pa abale ace, ndi m'nyumba yace.
5 Ndipo kumeneko sanakhoza Iye kucita zamphamvu konse, koma kuti anaika manja ace pa anthu odwala owerengeka, nawaciritsa.
6 Ndipo anazizwa cifukwa ca kusakhulupirira kwao. Ndipo anayendayenda m'midzi yozungulirapo, naphunzitsa.
7 Ndipo anadziitanira khumi ndi awiriwo, nayamba kuwatumiza Iwo awiri awiri; nawapatsa mphamvu pa mizimu yonyansa;
8 ndipo anawauza kuti asatenge kanthu ka paulendo, koma ndodo yokha; asatenge mkate, kapena thumba, kapena ndalama m'lamba lao;
9 koma abvale nsapato; ndipo anati, Musabvale malaya awiri.
10 Ndipo ananena nao, Kumene kuli konse mukalowa m'nyumba, khalani komweko kufikira mukacokako.
11 Ndipo pamalo ponse sakulandirani, kapena kumvera inu, pakucoka kumeneko, sansani pfumbi liri ku mapazi anu, likhale mboni ya kwa iwo.
12 Ndipo anaturuka nalalikira kuti anthu atembenuke mitima.
13 Ndipo anaturutsa mizimu yoipa yambiri, nadzoza mafuta anthu ambiri akudwala, nawaciritsa.
14 Ndipo mfumu Herode anamva izi; pakuti dzina lace lidamveka; ndipo ananena, kuti, Yohane Mbatizi wauka kwa akufa, ndipo cifukwa cace mphamvu izi zicitacita mwa Iye.
15 Koma ena ananena, kuti, Ndiye Eliya, Anati enanso, Ndiye mneneri, monga ngati mmodzi wa aneneriwo,
16 Koma Herode pamene anamva, ananena, Yohane amene ndamdula mutu, wauka iyeyo.
17 Pakuti Herode, mwini yekha, adatuma anthu namgwira Yohane, nammanga m'nyumba yandende, cifukwa ca Herodiya, mkazi wa Filipo mbale wace; cifukwa adamkwatira iye.
18 Pakuti Yohane adanena kwa Herode, Si kuloledwa kwa inu kukhala naye mkazi wa mbale wanu.
19 Ndipo Herodiya anamuda, nafuna kumupha; koma sanakhoza;
20 pakuti Herode anaopa Yohane, podziwa kuti ali munthu wolungama ndi woyera mtima, ndipo anamsunga iye. Ndipo pamene anamva iye anathedwa nzeru, oakondwa kumva iye.
21 Ndipo pamene panafika tsiku loyenera, tsiku la kubadwa kwace kwa Herode, iye anawakonzera phwando akuru ace ndi akazembe ace ndi anthu omveka a ku Galileya;
22 ndipo pamene mwana wamkazi wa Herodiya analowa yekha nabvina, anakondwetsa Herode ndi iwo akukhala naye pacakudya; ndipo mfumuyo inati kwa buthulo, Tapempha kwa ine ciri conse ucifuna, ndidzakupatsa iwe.
23 Ndipo anamlumbirira iye, kuti, Ciri conse ukandipempha ndidzakupatsa, kungakhale kukugawira ufumu wanga.
24 Ndipo anaturuka, nati kwa amace, Ndidzapempha ciani? Ndipo iyel anati, Mutu wace wa Yohane Mbatizi.
25 Ndipo pomwepo analowa m'mangu m'mangu kwa mfumu, napempha kuti, Ndifuna kuti mundipatse tsopano apa, mutu wace wa Yohane Mbatizi mumbizi.
26 Ndipo mfumu inamva cisoni cacikuru; koma cifukwa ca malumbiro ace, ndi ca iwo akukhala pacakudya, sanafuna kumkaniza.
27 Ndipo pomwepo mfumu inatuma mnyamata, namlamulira akatenge mutu wace; ndipo iye anamuka namdula mutu m'nyumba yandende;
28 natengera mutu wace mumbizi, naupereka kwa buthulo; ndipo buthu linaupereka kwa amace.
29 Ndipo m'mene ophunzira ace anamva, anadza nanyamula mtembo wace nauika m'manda.
30 Ndipo atumwi anasonkhana kwa Yesu; namuuza ziri zonse adazicita, ndi zonse adaziphunzitsa,
31 Ndipo Iye ananena nao, Idzani inu nokha padera ku malo acipululu, mupumule kamphindi, Pakuti akudza ndi akucoka anali piringu piringu, ndipo analibe nthawi yokwanira kudya.
32 Ndipo anacokera m'ngalawa kunka ku malo acipululu padera.
33 Ndipo anthu anawaona alikumuka, ndipo ambiri anawazindikila, nathamangira limodzi kumeneko pamtunda, ocokera m'midzi monse, nawapitirira.
34 Ndipo anaturuka Iye, naona khamu lalikuru la anthu, nagwidwa cifundo ndi iwo, cifukwa anali ngati nkhosa zopanda mbusa; ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.
35 Ndipo pamene dzuwa lidapendeka ndithu, anadza kwa Iye ophunzira ace, nanena, Malo ana nga cipululu, ndi dzuwa lapendeka ndithu;
36 muwauze kuti amuke, alowe kumiraga ndi ku midzi yozungulira, akadzigulire okha kanthu kakudya.
37 Koma Iye anayankha nati kwa iwo, Apatseni kudya ndinu. Ndipo iwo ananena naye, Kodi tikapita ife ndi kugula mikate ya pa marupiya atheka mazana awiri, ndi kuwapatsa kudya?
38 Ndipo Iye ananena nao, kuti, Muli nayo mikate ingati? pitani, mukaone. Ndipo m'mene anadziwa ananena, lsanu, ndi nsomba ziwiri.
39 Ndipo anawalamulira kuti akhalitse pansi onse magulu magulu pamsipu.
40 Ndipo anakhala pansi mabungwe mabungwe a makumi khumi, ndi a makumi asanu.
41 Ndipo Iye anatenga mikate isanuyo ndi nsomba ziwirizo nayang'anakumwamba, nadalitsa, nagawa mikate; napatsa kwa ophunzira kuti apereke kwa iwo; ndi nsomba ziwiri anagawira onsewo.
42 Ndipo anadya iwo onse, nakhuta.
43 Ndipo anatola makombo mitanga khumi ndi iwiri, ndiponso za nsomba.
44 Ndipo amene anadya mikate iyo anali amuna zikwi zisanu.
45 Ndipo pomwepo Iye anakangamiza ophunzira ace alowe rri'ngalawa, ndi kumtsogolera kutsidya lija ku Betsaida, m'mene Iye yekha alimkuuza khamulo kuti amuke.
46 Ndipo atalawirana nao, anacoka Iye, nalowa m'phiri kukapemphera,
47 Ndipo pofika madzulo ngalawa inali pakati pa nyanja, ndi Iye yekha pamtunda.
48 Ndipo pakuwaona ali kubvutidwa ndi kupalasa, pakuti mphepo inadza nikomana nao, pa uionda wacinai wa usiku Iye anadza kwa iwo, alikuyenda pamwamba pa nyanja; nati awapitirire;
49 koma iwo, pamene anamuona alikuyenda panyanja, anayesa kuti ndi mzukwa, napfuula:
50 pakuti iwo onse anamuona Iye, nanthunthumira. Koma pomwepo anawalankhula nanena nao, Limbani mtima; ndinetu, musaope,
51 Ndipo Iye anakwera, nalowa kwa iwo m'ngalawa, ndipo mphepo inaleka; ndipo anadabwa kwakukuru mwa iwo okha;
52 pakuti sanazindikira za mikateyo, kama mitima yao inauma.
53 Ndipo ataoloka iwo, anafika pamtunda ku Genesarete, nakoceza padooko.
54 Ndipo pamene anaturuka m'ngalawa anamzindikila pomwepo,
55 nathamangira dziko lonselo nayamba kunyamula anthu odwaia pa akama ao, kufika nao kumene anamva kuti analiko Iye.
56 Ndipo kumene konse adalowa Iye m'midzi, kapena m'mizinda, kapena m'miraga, anthu anagoneka odwala pamisika, 1 nampempha Iye kuti akakhudze ngakhale mphonje yokha ya cobvala cace; ndipo onse amene anamkhudza anaciritsidwa.
1 Ndipo anasonkhana kwa Iye Afarisi, ndi alembi ena, akucokera ku Yerusalemu,
2 ndipo anaona kuti ophunzira ace ena anadya mkate ndi m'manja mwakuda, ndiwo osasamba.
3 Pakuti Afarisi, ndi Ayuda onse sakudya osasamba m'manja ao, kuti asungire mwambo wa akuru;
4 ndipo pakucoka kumsika, sakudya osasamba m'thupi; ndipo ziripo zinthu zina zambiri anazilandira kuzisunga, ndizo matsukidwe a zikho, ndi miphika, ndi zotengera zamkuwa.
5 Ndipo Afarisi ndi alembi anamfunsa Iye, kuti, Bwanji ophunzira anu satsata mwambo wa akuru, koma akudya mkate wao ndi m'manja mwakuda?
6 Ndipo Iye ananena nao, Yesaya ananenera bwino za inu onyenga, monga mwalembedwa, Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao, Koma mtima wao ukhala kutari ndi ine.
7 Koma andilambira Ine kwacabe, Ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.
8 Musiya lamulo la Mulungu, nimusunga mwambo wa anthu.
9 Ndipo ananena nao, Bwino mukaniza lamulo la Mulungu, kuti musunge mwambo wanu,
10 Pakuti Mose anati, Lemekeza atate wako ndi amako; ndipo iye wakunenera zotpa atate wace kapena amai wace, afe ndithu;
11 koma inu munena, Munthu akati kwa atate wace, kapena amai wace, Karban, ndiko kuti Mtulo, cimene ukadathandizidwa naco ndi ine,
12 simulolanso kumcitira kanthu atate wace kapena amai wace;
13 muyesa acabe mau a Mulungu mwa mwambo wanu, umene munaupereka: ndi zinthu zotere zambiri muzicita.
14 Ndipo anadziitaniranso khamu la anthu, nanena nao, Mverani Ine nonsenu, ndipo dziwitsani:
15 kulibe kanthu kunja kwa munthu kakulowa mwa iye, kangathe kumdetsa: koma zinthu zakuturuka mwa munthu, ndizo zakumdetsa munthu.[
16 ]
17 Ndipo m'mene Iye adalowa m'nyumba kusiyana ndi khamulo, ophunzira ace anamfunsa Iye faruzolo.
18 Ndipo ananena nao, Mutero inunso opanda nzeru kodi? Kodi simuzindikira kuti kanthu kali konse kocokera kunja kakulowa mwa munthu, sikangathe kumdetsa iye;
19 cifukwa sikalowa mumtima mwace, koma m'mimba mwace, ndipo katurukira kuthengo? Ndipo potero anayeretsa zakudya zonse.
20 Ndipo anati, Coturuka mwa munthu ndico cidetsa munthu.
21 Pakuti m'kati mwace mwa mitima ya anthu, muturuka maganizo oipa, zaciwerewere,
22 zakuba, zakupha, zacigololo, masiriro, zoipa, cinyengo, cinyanso, diso loipa, mwano, kudzikuza, kupusa:
23 zoipa izi zonse zituruka m'kati, nizidetsa munthu.
24 Ndipo Iye anauka nacoka kumeneko, nanka ku maiko a ku Turo ndi Sidoni, Ndipo analowa m'nyumba, nafuna kuti asadziwe anthu; ndipo sanakhoza kubisika.
25 Koma pomwepo mkazi, kabuthu kace kanali ndi mzimu wonyansa, pamene anamva za Iye, anadza, nagwa pa mapazi ace.
26 Koma mkaziyo anali Mhelene, mtundu wace MsuroFonika. Ndipo anampempha Iye kuti aturutse ciwanda m'mwana wace.
27 Ndipo ananena naye, Baleka, athange akhuta ana; pakuti si kwabwino kuti titenge mkate wa ana ndi kuutayira tiagaru,
28 Koma iye anabvomera nanena ndi Iye, inde Ambuye; tingakhale tiagaru ta pansi pa gome tikudyako nyenyeswa za ana.
29 Ndipo anati kwa iye, Cifukwa ca mau amene, muka; ciwanda caturuka m'mwana wako wamkazi.
30 Ndipo anacoka kunka kunyumba kwace, napeza mwana atamgoneka pakama, ndi ciwanda citaturuka.
31 Ndipo anaturukanso m'maiko a ku Turo, nadzera pakati pa Sidoni, cufikira ku nyanja ya Galileya, ndi cupyola pakati pa maiko a ku Dekapolio
32 Ndipo anadza naye kwa Iye munthu wogontha, ndi wacibwibwi; ndipo anampempha Iye kuti aike dzanja pa iye.
33 Ndipo anampatula pa khamu la anthu pa yekha, nalonga zala zace m'makutu mwace, nalabvula malobvu, nakhudza lilime lace:
34 nagadamira kumwamba, nausa moyo, nanena naye, Elata, ndiko, Tatseguka.
35 Ndipo makutu ace anatseguka, ndi comangira lilime lace cinamasulidwa, ndipo analankhula cilunjikire.
36 Ndipo anawalamulira kuti asauze munthu, ali yense; koma monga momwe Iye anawalamulitsa momwenso makamaka analalikira kopambana.
37 Ndipo anadabwa kwakukurukuru, nanena, Wacita Iye zonse bwino; angakhale ogontha awamvetsa, ndi osalankhula awalankhulitsa.
1 Masiku ajawo pakukhalanso khamu lalikuru la anthu, ndipo analibe kanthu kakudya, iye anadziitanira ophunzira ace, nanena nao,
2 Ndimva nalo cifundo khamulo, cifukwa ali ndi Ine cikhalire masiku atatu, ndipo alibe kanthu kakudya:
3 ndipo ngati ndiwauza iwo amuke kwao osadya kanthu, adzakomoka panjira; ndipo ena iwo acokera kutali.
4 Ndipo ophunzira ace anamyankha Iye, kuti, Munthu adzatha kutenga kuti mikate yakukhutitsa anthu awa m'cipululu muno?
5 Ndipo anawafunsa, Muli nayo mikate ingati? Ndipo anati, Isanu ndi iwiri.
6 Ndipo analamulira anthu a khamulo akhale pansi; natenga mikate isanu ndi iwiriyo, nayamika, nanyema, napatsa ophunzira ace, kuti apereke kwa iwo; ndipo anapereka kwa khamulo.
7 Ndipo anali nato tinsomba towerengeka; ndipo Iye anatidalitsa, nati atipereke itonso.
8 Ndipo anadya nakhuta; ndipo anatola makombo malicero asanu ndi awiri.
9 Ndipo iwo anali ngati zikwi zinai; ndipo Iye analawirana nao.
10 Ndipo pomwepo analowa m'ngaiawa ndi akhupunzira ace, nafika ku mbali ya ku Dalmanuta.
11 Ndipo Afarisi anaturuka, nayamba kufunsana naye, ndi kufuna kwa Iye cizindikilo cocokera Kumwamba, namuyesa Iye.
12 Ndipo anausitsa moyo m'mzimu wace, nanena, Anthu a mbadwo uno afunafuna cizindikilo bwanji? indetu ndinena kwa inu, ngati cizindikilo cidzapatsidwa kwa mbadwo uno!
13 Ndipo anawasiya iwo, nalowanso m'ngalawa, nacoka kunka ku tsidya lija.
14 Ndipo ophunzira adaiwala kutenga mikate, ndipo analibe mkate m'ngalawa koma umodzi wokha.
15 Ndipo Iye anawalamula, nanena, Yang'anirani, penyani kuti mupewe cotupitsa mkate ca Afarisi, ndi cotupitsa mkate ca Herode.
16 Ndipo anatsutsana wina ndi mnzace, nanena kuti, Tiribe mikate.
17 Ndipo Yesu pamene anazindikira, ananena nao, Bwanji mutsutsana cifukwa mulibe mkate? kodi kufikira tsopano simuzindikira, nisimudziwitsa? kodi muli nayo mitima yanu youma?
18 Pokhala nao maso simupenya kodi? ndi pokhala nao makutu simukumva kodi? ndipo simukumbukila kodi?
19 Pamene ndinawagawira anthu zikwi zisanu mikate isanu ija, munatola mitanga ingati yodzala ndi makombo? Ananena naye, Khumi ndi iwiri.
20 Ndipo mikate isanu ndi iwiri kwa anthu zikwi zinai, munatola malicero angati odzala ndi makombo? Ndipo ananena naye, Asanu ndi awiri.
21 Ndipo Iye ananena nao, Simudziwitsa ngakhale tsopano kodi?
22 Ndipo anadza ku Betsaida. Ndipo anadza naye kwa Iye munthu wakhungu, nampempha Iye kuti amkhudze.
23 Ndipo anamgwira dzanja munthu wakhunguyo, naturukira naye kunja kwa mudzi; ndipo atamthira malobvu m'maso mwace, naika manja pa iye, anamfunsa, Uona kanthu kodi?
24 Ndipo anakweza maso, nanena, Ndiona anthu; pakuti ndiwapenya ayendayenda ngati mitengo.
25 Pamenepo anaikanso manja m'maso mwace; ndipo anapenyetsa, naciritsidwa, naona zonse mbee.
26 Ndipo anamtumiza amuke kwao, nanena, Usalowe konse m'mudzi.
27 Ndipo anaturuka Yesu, ndi ophunzira ace, nalowa ku midzi ya ku Kaisareya wa Filipi; ndipo panjira anafunsa ophunzira ace, nanena nao, Kodi anthu anena kuti Ine ndine yani?
28 Ndipo ananena, nati, Yohane Mbatizi; ndi ena, Eliya; koma ena, Mmodzi wa aneneri.
29 Ndipo Iye anawafunsa, Koma inu munena kuti ndine yani? Petro anayankha nanena naye, Ndinu Kristu.
30 Ndipo anawauzitsa iwo kuti asanene kwa munthu mmodzi za Iye.
31 Ndipo anayamba kuwaphunzitsa, kuti kuyenera kuti Mwana wa munthu akamve zowawa zambiri, nakakanidwe ndi akuru ndi ansembe akulu, ndi alembi, nakaphedwe, ndipo mkuca wace akauke.
32 Ndipo mauwo ananena poyera. Ndipo Petro anamtenga Iye, nayamba kumdzudzula.
33 Koma Iye anapotoloka, napenya ophunzira ace, namdzudzula Petro, nanena, Coka, pita kumbuyo kwanga, Satana iwe; popeza susamalira zinthu za Mulungu, koma za anthu.
34 Ndipo anadziitanira khamulo la anthu pamodzi ndi ophunzira ace, nati kwa iwo, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikanize yekha, nanyamule mtanda wace, nanditsate Ine.
35 Pakuti yense wakufuna kupulumutsa moyo wace adzautaya; ndipo yense wakutaya moyo wace cifukwa ca Ine, ndi cifukwa ca Uthenga Wabwino, adzaupulumutsa.
36 Pakuti munthu apindulanji akadzilemezera dziko lonse, natayapo moyo wace?
37 Pakuti munthu akapereka ciani cosintha naco moyo wace?
38 Pakuti yense wakucita manyazi cifukwa ca Ine, ndi ca mau anga mu mbadwo uno wacigololo ndi wocimwa, Mwana wa munthu adzacitanso manyazi cifukwa ca iyeyu, pamene Iye adzafika nao angelo ace oyera, mu ulemerero wa Atate wace.
1 Ndipo ananena nao, Ndithu ndinena ndi inu kuti, Alipo ena akuimirira pano, amene sadzalawa imfa konse, kufikira akaona Ufumu wa Mulungu utadza ndi mphamvu.
2 Ndipo atapita masiku asanu ndi limodzi, Yesu anatenga Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane, nakwera nao pa phiri lalitali padera pa okha; ndipo anasandulika pamaso pao:
3 ndipo zobvala zace zinakhala zonyezimira, zoyera mbu; monga ngati muomba wotsuka nsaru pa dziko lapansi sangathe kuziyeretsai.
4 Ndipo anaonekera kwa iwo Eliya ndi Mose, alikulankhulana ndi Yesu.
5 Ndipo Petro anayankha, nanena ndi Yesu, Rabi, kutikomera ife kukhala pano; ndipo timange misasa itatu; umodzi wa inu, ndi wina wa Mose, ndi wina wa Eliya.
6 Pakuti sanadziwa cimene adzayankha; cifukwa anacita mantha ndithu.
7 Ndipo panadza mtambo wakuwaphimba iwo; ndipo mau munaturuka m'mtambomo, kuti, Uyu ndiye Mwana wanga wokondedwa; mverani Iye.
8 Ndipo dzidzidzi pounguzaunguza, sanapenya munthu wina yense, koma Yesu yekha, ndi iwo eni.
9 Ndipo pakutsika iwo paphiri, Iye anawalamulira kuti asauze munthu zinthu zimene adaziona, koma pamene Mwana wa munthu akadzauka kwa akufa ndipo.
10 Ndipo anasunga mauwo, nafunsana mwa iwo okha, kuti, Kuuka kwa akufa nciani?
11 Ndipo anamfunsa Iye, nanena, Nanga alembi anena kuti adzayamba kufika Eliya?
12 Ndipo Iye ananena nao, Eliya ayamba kudza ndithu, nadzakonza zinthu zonse; ndipo kwalembedwa bwanji za Mwana wa munthu, kuti ayenera kumva zowawa zambiri ndi kuyesedwa cabe?
13 Koma ndinena ndi inu kuti anafikadi Eliya, ndipo anamcitiranso ziri zonse iwo anazifuna, monga kwalembedwa za iye.
14 Ndipo pamene anadza kwa ophunzira, anaona khamu lalikuru la anthu ozungulira iwo, ndi alembi alikufunsana nao.
15 Ndipo pomwepo anthu onse a khamulo, pakumuona Iye, anazizwa kwambiri, namthamangira Iye, namlankhula.
16 Ndipo anawafunsa iwo, Mufunsa na nao ciani?
17 Ndipo wina wa m'khamulo anamyankha Iye, kuti, Mphunzitsi, ndadza naye kwa Inu mwana wanga, ali nao mzimu wosalankhula;
18 ndipo ponse pamene umgwira, umgwetsa; ndipo acita thobvu, nakukuta mano, nanyololoka; ndipo ndinalankhula nao ophunzira anu kuti auturutse; koma sanakhoza.
19 Ndipo Iye anawayankha nanena, Mbadwo wosakhulupirira inu, ndidzakhala ndi inu kufikira liti? ndidzakulekererani nthawi yanji? Mudze naye kwa Ine.
20 Ndipo anadza naye kwa Iye; ndipo pakumuona, pomwepo mzimuwo unamng'amba koopsya; ndipo anagwa pansi nabvimbvinika ndi kucita thobvu.
21 Ndipo Iye anafunsa atate wace, kuti, Cimeneci cinayamba kumgwira liti? Ndipo anati, Cidamyamba akali mwana.
22 Ndipo kawiri kawiri ukamtaya kumoto ndi kumadzi, kumuononga; koma ngati mukhoza kucita kanthu mtithandize, ndi kuticitira cifundo.
23 Ndipo Yesu ananena naye, Ngati mukhoza! Zinthu zonse zitheka ndi iye wakukhulupirira.
24 Pomwepo atate wa mwana anapfuula, nanena, Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga.
25 Ndipo pamene Yesu anaona kuti khamu la anthu lirikuthamangira pamodzi, anadzudzula mzimu woipawo, nanena ndi uwo, Mzimu wosalankhula ndi wogontha iwe, Ine ndikulamula iwe, turuka mwa iye, ndipo usalowenso mwa iye.
26 Ndipo pamene unapfuula, numng'ambitsa, unaturuka; ndipo mwana anakhala ngati wakufa; kotero kuti ambiri ananena, Wamwalira.
27 Koma Yesu anamgwira dzanja lace, namnyamutsa; ndipo anaimirira.
28 Ndipo pamene Iye adalowa m'nyumba, ophunzira ace anamfunsa m'tseri, kuti, Nanga bwanji sitinakhoza ife kuuturutsa?
29 Ndipo Iye anati kwa iwo, Mtundu uwu sukhoza kuturuka ndi kanthu kena konse, koma ndi kupemphera.
30 Ndipo anacoka iwo kumeneko, napyola pakati pa Galileya; ndipo Iye sanafuna kuti munthu adziwe.
31 Pakuti anaphunzitsa ophunzira ace, nanena nao, kuti, Mwana wa munthu aperekedwa m'manja a anthu, ndipo adzamupha Iye; ndipo ataphedwa, adzauka pofika masiku atatu.
32 Koma iwo sanazindikira mauwo, naopa kumfunsa.
33 Ndipo iwo anadza ku Kapernao; ndipo pamene anakhala m'nyumba, Iye anawafunsa, Munalikutsutsana ninji panjira?
34 Koma iwo anakhala cete; pakuti anatsutsana wina ndi mnzace panjira, kuti, wamkuru ndani?
35 Ndipo m'mene anakhala pansi anaitana khumi ndi awiriwo; nanena nao, Ngati munthu afuna kukhala woyamba, akhale wakuthungo wa onse, ndi mtumiki wa onse.
36 Ndipo anatenga kamwana, nakaika pakati pao, nakayangata, nanena nao,
37 Munthu ali yense adzalandira kamodzi ka tiana totere cifukwa ca dzina langa, alandira ine; ndipo yense amene akalandira Ine, salandira Ine, koma Iye amene anandituma Ine.
38 Yohane anati kwa Iye, Mphunzitsi, tinaona munthu alikuturutsa ziwanda m'dzina lanu; ndipo tinamletsa, cifukwa sanalikutsata ife.
39 Koma Yesu anati, Musamamletsa iye; pakuti palibe munthu adzacita camphamvu m'dzina langa, nadzakhoza msanga kundinenera Ine zoipa.
40 Pakuti iye wosatsutsana ndi ife athandizana nafe.
41 Pakuti munthu ali yense adzakumwetsani inu cikho ca madzi m'dzina langa cifukwa muli ace a Kristu, indetu ndinena ndi inu, kuti iye sadzataya konse mphotho yace.
42 Ndipo yense amene adzalakwitsa kamodzi ka tiana timeneto takukhulupirira Ine, kuli kwabwino kwa iye makamaka kuti mwala waukuru wamphero ukolowekedwe m'khosi mwace, naponyedwe iye m'nyanja.
43 Ndipo ngati dzanja lako likulakwitsa iwe, ulidule: nkwabwino kwa iwe kulowa m'moyo wopunduka dzanja, koposa kukhala ndi manja ako awiri ndi kulowa m'gehena, m'moto wosazima.[
44 ]
45 Ndipo ngati phazi lako likulakwitsa, ulidule; kulowa iwe m'moyo wopunduka mwendo, kuli kwabwino koposa ndi kukhala ndi mapazi ako awiri ndi kuponyedwa m'gehena.[
46 ]
47 Ndipo ngati diso lako likulakwitsa ulikolowole; kulowa iwe m'Ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi kuli kwabwino koposa ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa m'gehena;
48 kumeneko mphutsi yao siikufa, ndi mota suzimidwa.
49 Pakuti onse adzathiridwa mcere wamoto,
50 Mcere uli wabwino; koma ngati mcere unasukuluka, mudzaukoleretsa ndi ciani? Khalani nao mcere mwa inu nokha, ndipo khalani ndi mtendere wina ndi mnzace.
1 Ndipo ananyamuka Iye kumeneko, nadza ku maiko a ku Yudeya ndi ku tsidya lija la Yordano; ndipo anasonkhananso kwa Iye makamu a anthu; ndipo monga anazolowera, anawaphunzitsanso.
2 Ndipo anadza kwa Iye Afarisi, namfunsa Iye ngati kuloledwa kuti munthu acotse mkazi wace, namuyesa Iye.
3 Ndipo Iye anayankha nati kwa iwo, Kodi Mose anakulamulirani ciani?
4 Ndipo anati, Mose analola kulembera kalata wakulekanira, ndi kumcotsa.
5 Koma Yesu anati kwa iwo, Cifukwa ca kuuma kwa mitima yanu anakulemberani lamulo ili.
6 Koma kuyambira pa ciyambi ca malengedwe anawapanga mwamuna ndi mkazi.
7 Cifukwa cace mwamuna adzasiya atate wace ndi amai wace, ndipo adzaphatikizana ndi mkazi wace;
8 ndipo awiriwa adzakhala thupi limodzi: kotero kuti salinso awiri, koma thupi limodzi.
9 Cifukwa cace cimene Mulungu anacimanga pamodzi, asacilekanitse munthu.
10 Ndipo m'nyumba ophunzira anamfunsanso za cinthu ici.
11 Ndipo Iye ananena nao, Munthu ali yense akacotsa mkazi wace, nakakwatira wina, acita cigololo kulakwira mkaziyo;
12 ndipo ngati mkazi akacotsa mwamuna wace, nakwatiwa ndi wina, acita cigololo iyeyu.
13 Ndipo analinkudza nato kwa Iye tiana, kuti akatikhudze; ndipo ophunzirawo anawadzudzula.
14 Koma pamene Yesu anaona anakwiya, ndipo anati kwa iwo, Lolani tiana tidze kwa Ine; musatiletse: pakuti Ufumu wa Mulungu uli wa totere.
15 Ndithu ndinena ndi inu, Munthu ali yense wosalandira Ufumu wa Mulungu ngati kamwana, sadzalowamo konse.
16 Ndipo Iye anatiyangata, natidalitsa, ndi kuika manja ace pa ito.
17 Ndipo pamene Iye anaturuka kutsata njira, anamthamangira munthu, namgwadira Iye, namfunsa, Mphunzitsi wabwino, ndidzacita ciani kuti ndilandire moyo wosatha?
18 Ndipo Yesu anati kwa iye, Undicha Ine wabwino bwanji? palibe wabwino koma mmodzi, ndiye Mulungu.
19 Udziwa malamulo: Usaphe, Usacite cigololo, Usabe, Usacite umboni wakunama, Usanyenge, Lemekeza atate wako ndi amako.
20 Ndipo iye anati kwa Iye, Mphunzitsi, zonsezi ndinazisunga kuyambira ndiri mwana.
21 Ndipo Yesu anamyang'ana, namkonda, nati kwa iye, Cinthu cimodzi cikusowa: pita, gulitsa zonse uli nazo, nuzipereke kwa anthu aumphawi, ndipo cuma udzakhala naco m'mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.
22 Koma nkhope yace inagwa pa mau awa, ndipo anacoka iye wacisoni; pakuti anali mwini cuma cambiri.
23 Ndipo Yesu anaunguzaunguza, nanena ndi ophunzira ace, Okhala naco cuma adzalowa mu Ufumu wa Mulungu ndi kubvuta nanga!
24 Ndipo ophunzirawo anazizwa ndithu ndi mau ace. Koma Yesu anayankhanso nanena nao, Ananu, nkobvuta ndithu kwa iwo akutama cuma kulowa mu Ufumu wa Mulungu!
25 Nkwa pafupi kuti ngamila ipyole diso la singano koposa kuti mwini cuma alowe mu Ufumu wa Mulungu.
26 Ndipo anadabwa, nanena kwa Iye, Ndipo angathe kupulumuka ndani?
27 Yesu anawayang'ana iwo nati, Sikutheka ndi anthu, koma kutheka ndi Mulungu; pakuti zinthu zonse zitheka ndi Mulungu.
28 Petro anayamba kunena naye, Onani, ife tinasiya zonse, ndipo tinakutsatani Inu.
29 Yesu anati, Ndinena ndi inu ndithu, Palibe munthu anasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena amai, kapena atate, kapena ana, kapena minda, cifukwa ca Ine, ndi cifukwa ca Uthenga Wabwinowo,
30 amene sadzalandira makumi khumi tsopano nthawi yino, nyumba, ndi abale, ndi alongo, ndi amai, ndi ana, ndi minda, pamodzi ndi mazunzo; ndipo nthawi irinkudza, moyo wosatha.
31 Koma ambiri akuyamba adzakhala akuthungo, ndi akuthungo adzakhala oyamba.
32 Ndipo iwo anali m'njira alinkukwera kunka ku Yerusalemu; ndipo Yesu analikuwatsogolera; ndipo iwo anazizwa; ndipo akumtsatawo anacita mantha. Ndipo Iye anatenganso khumi ndi awiriwo, nayamba kuwauza zinthu zimene zidzamfikira Iye,
33 nati, Taonani, tikwera ku Yerusalemu; ndipo Mwana wa munthu adzaperekedwa kwa ansembe akuru ndi alembi; ndipo iwo adzamweruza kuti ayenera imfa, nadzampereka Iye kwa anthu a mitundu;
34 ndipo adzamnyoza Iye, nadzamthira malobvu, nadzamkwapula Iye, nadzamupha; ndipo pofika masiku atatu adzauka.
35 Ndipo anadza kwa Iye Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, nanena naye, Mphunzitsi, tifuna kuti mudzaticitire cimene ciri conse tidzapempha kwa Inu.
36 Ndipo Iye anati kwa iwo, Mufuna kuti ndidzakucitireni inu ciani?
37 Ndipo iwo anati kwa Iye, Mutipatse ife kuti tikhale mmodzi ku dzanja lanu lamanja, ndi wina kulamanzere, m'ulemerero wanu.
38 Koma Yesu anati kwa iwo, Simudziwa cimene mucipempha, Mukhoza kodi kumwera cikho cimene ndimwera Ine? kapena kubatizidwa ndi ubatizo umene ndibatizidwa nao Ine?
39 Ndipo anati kwa Iye, Tikhoza. Ndipo Yesu anati kwa iwo, Cikho cimene ndimwera Ine mudzamwera; ndipo ubatizo umene ndibatizidwa nao Ine, mudzabatizidwa nao;
40 koma kukhala ku dzanja langa lamanja, kapena kulamanzere sikuli kwanga kupatsa; koma kuli kwa iwo amene adawakonzeratu,
41 Ndipo pamene khumiwo anamva, anayamba kupsa mtima cifukwa ca Yakobo ndi Yohane.
42 Ndipo Yesu anawaitana, nanena nao, Mudziwa kuti iwo amene ayesedwa ambuye a mitundu ya anthu amacita ufumu pa iwo; ndipo akuru ao amacita ulamuliro pa iwo.
43 Koma mwa inu sikutero ai; kama amene ali yense afuna kukhala wamkuru mwa inu adzakhala mtumiki wanu;
44 ndipo amene ali yense afuna kukhala woyamba mwa inu adzakhala kapolo wa onse.
45 Pakuti ndithu, Mwana wa munthu sanadza kutumikiridwa, koma kutumikira, ndi kupereka moyo wace dipo la kwa anthu ambiri.
46 Ndipo iwo anafika ku Yeriko; ndipo m'mene Iye analikuturuka m'Yeriko, ndi ophunzira ace, ndi khamu lalikuru la anthu, mwana wa Timeyu, Bartimeyu, wopempha wakhungu, analikukhala pansi m'mbali mwa njira.
47 Ndipo pamene anamva kuti ndi Yesu wa ku Nazarete, anayamba kupfuula, ndi kunena, Yesu, Inu Mwana wa Davide, mundicitire ine cifundo.
48 Ndipo ambiri anamuyamula kuti atonthole: koma makamaka anapfuulitsa kuti, Inu Mwana wa Davide, mundicitire cifundo.
49 Ndipo Yesu anaima, nati, Mwitaneni. Ndipo anaitana wakhunguyo, nanena naye, Limba mtima; nyamuka, akuitana.
50 Ndipo iye anataya copfunda cace, nazunzuka, nadza kwa Yesu.
51 Ndipo Yesu anamyankha, nati, Ufuna kuti ndikucitire ciani? Ndipo wakhunguyo anati kwa Iye, Raboni, ndilandire kuona kwanga.
52 Ndipo Yesu anati kwa iye, Muka; cikhulupiriro cako cakupulumutsa iwe. Ndipo pomwepo anapenyanso; namtsata Iye panjira.
1 Ndipo pamene iwo anayandikira ku Yerusalemu, ku Betefage ndi Betaniya, pa phiri la Azitona, anatuma awiri a ophunzira ace,
2 nanena nao, Mukani, lowani m'mudzi wapandunji ndi inu; ndipo pomwepo pakulowamo mudzapeza mwana wa buru womangidwa, amene palibe munthu anakhalapo kale lonse; mmasuleni, ndipo mubwere naye.
3 Ndipo munthu akati kwa inu, Mutero bwanji? Katini, Ambuye amfuna iye; ndipo pomwepo adzamtumiza kuno.
4 Ndipo anacoka, napeza mwana wa buru womangidwa pakhomo, pabwalo m'khwalala, nammasula iye.
5 Ndipo ena akuima kumeneko ananena nao, Mucita ciani ndi kumasula mwana wa buru?
6 Ndipo anati kwa iwo monga momwe ananena Yesu: ndipo anawalola iwo apite naye.
7 Ndipo anabwera naye mwana wa buru kwa Yesu, naika zobvala zao pa iye, ndipo Iye anakhala pamenepo.
8 Ndimo ambiri anayala zobvala zao panjira; ndi ena zitsamba, anazidula m'minda.
9 Ndipo akutsogolera, ndi iwo akutsata, anapfuula, Hosana; Wolemekezeka Iye wakudza m'dzina la Ambuye:
10 Wolemekezeka Ufumu ulinkudza, wa atate wathu Davide; Hosana m'Kumwamba-mwamba.
11 Ndipo Iye analowa m'Yerusalemu, m'Kacisi; ndipo m'mene anaunguza zinthu zonse, popeza ndi madzulo, anaturuka kupita ku Betaniya pamodzi ndi khumi ndi awiriwoo.
12 Ndipo m'mawa mwace, ataturuka ku Betaniya, Iye anamva njala.
13 Ndipo anaona mkuyu kutali, uli ndi masamba; ndipo anadza Iye, kuti kapena akapezapo kanthu: ndipo m'mene anafikako anapeza palibe kanthu koma masamba okha; pakuti siinali nyengo yace ya nkhuyu.
14 Ndipo anayankha nanena ndi uwo, Munthu sadzadyanso zipatso zako nthawi zonse. Ndipo ophunzira ace anamva,
15 Ndipo anafika iwo ku Yerusalemu; ndipo Iye analowa m'Kacisi, nayamba kuturutsa akugulitsa ndi akugula malonda m'Kacisimo, nagubuduza magome a osinthana ndalama, ndi mipando yaogulitsa nkhunda;
16 ndipo sanalola munthu ali yense kunyamula cotengera kupyola pakati pa Kacisi.
17 Ndipo anaphunzitsa, nanena nao, Sicilembedwa kodi, Nyumba yanga idzachedwa nyumba yakupempheramo anthu a mitundu yonse? koma inu mwaiyesa phanga la acifwamba.
18 Ndipo ansembe akuru ndi alembi anamva, nafunafuna momuonongera Iye; pakuti anamuopa, cifukwa khamu lonse la anthu linazizwa ndi ciphunzitso cace.
19 Ndipo masiku onse madzulo anaturuka Iye m'mudzi.
20 Ndipo m'mene anapitapo m'mawa mwace, anaona kuti mkuyu uja unafota, kuyambira kumizu.
21 Ndipo Petro anakumbukila, nanena naye, Rabi, onani, wafota mkuyuwo munautemberera.
22 Ndipo Yesu anayankha nanena nao, Khulupirirani Mulungu,
23 Ndithu ndinena ndi inu, kuti, Munthu ali yense akanena ndi phiri ili, Tanyamulidwa, nuponyedwe m'nyanja; wosakayika mumtima mwace, koma adzakhulupirira kuti cimene acinena cicitidwa, adzakhala naco.
24 Cifukwa cace ndinena ndi inu, Zinthu ziri zonse mukazipemphera ndi kuzipempha, khulupirirani kuti mwazilandira, ndipo mudzakhala nazo.
25 Ndipo pamene muimirira ndi kupemphera, kholulukirani, ngati munthu wakulakwirani kanthu; kuti Atate wanunso ali Kumwamba akhulolukire inu zolakwa zanu.
26
27 Ndipo iwo anadzanso ku Yerusalemu; ndipo m'mene Iye anali kuyenda m'Kacisi, anafika kwa Iye ansembe akuru, ndi alembi ndi akuru;
28 nanena naye, Izi muzicita ndi ulamuliro wotani? Kapena anakupatsani ndani ulamuliro uwu wakucita izi?
29 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ndikufunsani mau amodzi, mundiyankhe Ine, ndipo ndidzakuuzani ulamuliro umene ndicita nao zinthu zimenezi.
30 Ubatizo wa Yohane ucokera Kumwamba kodi, kapena kwa anthu? Mundiyankhe.
31 Ndipo anatsutsana mwa iwo okha, nanena, Tikati, Kumwamba; adzanena iye, Ndipo simunakhulupirira iye bwanji?
32 Koma tikati, Kwa anthu —anaopa anthuwo; pakuti onse anamuyesa Yohane mneneri ndithu.
33 Ndipo iwo anamyankha Yesu, nanena, Sitidziwa. Ndipo Yesu ananena nao, Inenso sindikuuzani ulamuliro umene ndicita nao zinthu zimenezi.
1 Ndipo Iye anayamba kulankhula nao m'mafanizo. Munthu analima munda wamphesa, nauzunguniza ndi linga, nakumba moponderamo mphesa, namanga nsanja, naukongoletsa kwa olima munda, namuka kwina.
2 Ndipo m'nyengo yace anatuma kapolo kwa olimawo, kuti alandireko kwa olimawo zipatso za m'munda wamphesa.
3 Ndipo iwo anamtenga iye, nampanda, namcotsa wopanda kanthu.
4 Ndipo anatumanso kapolo wina kwa iwo; ndipo ameneyu anamlasa mutu, namcitira zomcititsa manyazi.
5 Ndipo anatuma wina; iyeyu anamupha; ndi ena ambiri; ena anawapanda, ndi ena anawapha.
6 Anamtsalira mmodzi, ndiye mwana wace wokondedwa; potsiriza anamtuma iye kwa iwo, nanena, Adzamcitira ulemu mwana wanga.
7 Koma olima ajawo, ananena mwa iwo okha, Ameneyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe iye, ndipo mundawu udzakhala wathu.
8 Ndipo anamtenga, namupha iye, namtaya kunja kwa munda.
9 Pamenepo mwini munda adzacita ciani? Adzafika, nadzaononga olimawo, nadzapereka mundawo kwa ena.
10 Kodi simunawerenga ngakhale lembo ili; Mwala umene anaukana omanga nyumba, Womwewu unayesedwa mutu wa pangondya:
11 Ici cinacokera kwa Ambuye, Ndipo ciri cozizwitsa m'maso mwathu?
12 Ndipo anayesa kumgwira Iye; koma anaopa khamu la anthu, pakuti anazindikira kuti Iye anakamba fanizo ili kuwatsutsa iwo; ndipo anamsiya Iye, nacoka.
13 Ndipo anatuma kwa Iye ena a Afarisi ndi a Aherode, kuti akamkole Iye m'kulankhula kwace.
14 Ndipo pamene anafika, ananena naye, Mphunzitsi, tidziwa kuti muli woona, ndipo simusamala munthu; pakuti simuyang'ana nkhope ya anthu, koma muphunzitsa njira ya Mulungu moona: Nkuloleka kodi kupereka msonkho kwa Kaisara, kapena iai?
15 Kodi tipereke kapena tisapereke? Koma Iye anadziwa cinyengo cao, nati kwa iwo, Mundiyeseranji? Nditengereni rupiya latheka, kuti ndilione. Ndipo analitenga.
16 Ndipo ananena nao, Cithunzithunzi ici, ndi cilembo cace ziri za yani? Ndipo anati kwa Iye, Za Kaisara.
17 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Perekani zace za Kaisara kwa Kaisara, ndi zace za Mulungu kwa Mulungu. Ndipo anazizwa naye kwambiri.
18 Ndipo anadza kwa Iye Asaduki, amene amanena kuti palibe kuuka kwa akufa; ndipo anamfunsa Iye, nanena,
19 Mphunzitsi, Mose anatilembera, kuti, Akafa mbale wace wa munthu, nasiya mkazi, wosasiyapo mwana, mbale wace atenge mkazi wace, namuuldtsire mbale waceyo mbeu.
20 Analipo abale asanu ndi awiri; woyamba anakwatira mkazi, nafa, wosasiya mbeu;
21 ndipo waciwiri anamkwatira, nafa, wosasiya mbeu; ndipo wacitatunso anatero momwemo;
22 ndipo asanu ndi awiriwo analibe kusiya mbeu. Potsiriza pace pa onse mkazinso anafa.
23 Pakuuka adzakhala mkazi wa yani wa iwowa? Pakuti asanu ndi awiriwo adamuyesa mkazi wao.
24 Yesu ananena nao, Simusocera nanga mwa ici, popeza mulibe kudziwa malembo, kapena mphamvu yace ya Mulungu?
25 Pakuti pamene adzauka kwa akufa, sakwatira, kapena sakwatiwa; koma akhala ngati angelo a Kumwamba. Koma za akufa, kuti akauldtsidwa;
26 simunawerenga m'kalata wa Mose kodi, za Citsambaco, kuti Mulungu anati kwa iye, nanena, Ine Ndine Mulungu wa Abrahamu, ndi Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo?
27 Sali Mulungu wa akufa, koma wa amoyo: musocera inu ndithu.
28 Ndipo anadza mmodzi wa alembi, namva iwo alikufunsana pamodzi, ndipo pakudziwa kuti anawayankha bwino, anamfunsa Iye, Lamulo la m'tsogolo la onse ndi liti?
29 Yesu anayankha, kuti, La m'tsogolo ndili, Mvera, Israyeli; Ambuye Mulungu wathu, Ambuye ndiye mmodzi;
30 ndipouzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mphamvu yako yonse.
31 Laciwiri ndi ili, Uzikonda mnzako monga udzikonda mwini. Palibe lamulo lina lakuposa awa.
32 Ndipo mlembiyo anati kwa Iye, Cabwino, Mphunzitsi, mwanena zoona kuti ndiye mmodzi; ndipo palibe wina, koma Iye:
33 ndipo, kumkonda Iye ndi mtima wonse, ndi nzeru yonse, ndi mphamvu yonse, ndi kukonda mnzace monga adzikonda mwini, ndiko kuposa nsembe zopsereza zamphumphu zonse, ndi nsembe zophedwa.
34 Ndipo palmona kuti anayankha ndi nzeru, Yesu anati kwa iye, Suli kutali ndi Ufumu wa Mulungu. Ndipo palibe munthu analimbanso mtima kwnfunsa Iye kanthu.
35 Ndipo Yesu pamene anaphunzitsa m'Kacisi, anayankha, nanena, Bwanji alembi anena kuti Kristu ndiye mwana wa Davide?
36 Davide mwini yekha anati mwa Mzimu Woyera, Ambuye anati kwa Ambuye wanga, Khala ku dzanja langa lamanja, kufikira ndiwaika adani ako popondapo mapazi ako.
37 Davide mwini yekha amchula Iye Ambuye; ndipo ali mwana wace bwanji? Ndipo anthu a makamuwo anakondwa kumva Iye.
38 Ndipo m'ciphunzitso cace ananena, Yang'anirani mupewe alembi, akufuna kuyendayenda obvala miinjiro, ndi kulankhulidwa pamisika,
39 ndi kukhala nayo mipando yaulemu m'sunagoge, ndi malo aulemu pamapwando:
40 amenewo alusira nyumba za akazi amasiye, napemphera monyenga mau ambiri; amenewa adzalandira kulanga koposa.
41 Ndipo Iye anakhala pansi pandunji pa mosungiramo zopereka, napenya kuti khamu la anthu alikuponya ndalama mosungiramo; ndipo eni cuma ambiri anaponyamo zambiri.
42 Ndipo anadza mkazi wamasiye waumphawi, ndipo iye anaponyamo tindalama tiwiri tanng'ono tofa kakobiri kamodzi.
43 Ndipo anaitana ophunzira ace, nati kwa iwo, Ndithu ndinena ndi inu, Mkazi wamasiye amene waumphawi anaponya zambiri koposa onse akuponya mosungiramo:
44 pakuti anaponyamo onse mwa zocuruka zao; koma iye anaponya mwa kusowa kwace zonse anali nazo, inde moyo wace wonse.
1 Ndipo pamene analikuturuka Iye m'Kacisi, mmodzi wa ophunzira ace ananena kwa Iye, Mphunzitsi, onani, miyala yotere ndi nyumba yotere.
2 Ndipo Yesu anati kwa iye, Kodi waona nyumba izi zazikuru? Sudzasiyidwa pano mwala umodzi pamwamba pa unzace, umene sudzagwetsedwa.
3 Ndipo pamene anakhala Iye pa phiri la Azitona, popenyana ndi Kacisi, anamfunsa Iye m'tseri Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane, ndi Andreya, kuti,
4 Tiuzeni, zinthu izi zidzacitika liti? Ndi cotani cizindikilo cace cakuti ziri pafupi pa kumarizidwa zinthu izi zonse?
5 Ndipo Yesu anayamba kunena nao, Yang'anirani kuti munthu asakusoceretseni.
6 Ambiri adzafika m'dzina langa, nadzanena, Ine ndine Iye; nadzasoceretsa ambiri.
7 Ndipo m'mene mudzamva za nkhondo ndi mbiri zace za nkhondo, musamadera nkhawa: ziyenerakucitika izi; koma sicinafike cimariziro.
8 Pakuti mtundu wa anthu udzayambana ndi mtundu wina, ndipo ufumu ndi ufumu unzace: padzakhaia zibvomezi m'malo m'malo; padzakhala njala; izi ndi zoyambira za zowawa.
9 Koma inu mudziyang'anire inu nokha; pakuti adzakuperekani inu kwa akuru a mirandu; ndipo adzakukwapulani m'masunagoge; ndipo pamaso pa akazembe ndi mafwnu mudzaimirira cifukwa ca Ine, kukhale umboni kwa iwo.
10 Ndipo Uthenga Wabwino uyenera uyambe kulalikidwa kwa anthu a mitundu yonse.
11 Ndipo pamene adzapita nanu kumlandu, nadzakuperekani, musada nkhawa usanayambe mrandu ndi cimene mudzalankhula; koma ci mene cidzapatsidwa kwa inu m'mphindi yomweyo, mucilankhule; pakuti olankhula si ndinu, koma Mzimu Woyera.
12 Ndipo mbale adzapereka mbale wace kuti amuphe, ndi atate mwana wace; ndi ana adza yambana ndi akuwabala, nadzawaphetsa,
13 Ndipo adzada inu anthu onse cifukwa ca dzina langa: koma iye wakupirira kufikira cimariziro, yemweyo adzapulumutsidwa.
14 Ndipo pamene mukaona conyansa ca kupululutsa cirikuima pomwe siciyenera (wakuwerenga azindikile), pamenepo a m'Yudeya athawire kumapiri;
15 ndi iye amene ali pamwamba pa chindwi asatsike, kapena asalowe kukaturutsa kanthu m'nyumba mwace;
16 ndi iye amene ali kumunda asabwere kudzatenga Malaya ace.
17 Koma tsoka iwo akukhala ndi pakati, ndi akuyamwitsa ana masiku awol
18 Ndipo pempherani kuti kusakhale m'nyengo yacisanu.
19 Pakuti masiku aja padzakhala cisautso, conga sicinakhala cinzace kuyambira ciyambi ca cilengedwe cimene Mulungu anacilenga ndi kufikira tsopano, ndipo sicidzakhalanso nthawi zonse.
20 Ndipo Ambuye akadapanda kufupikitsa masikuwo, sakadapulumuka munthu mmodzi yense; koma cifukwa ca osankhidwa amene anawasankha, anafupikitsa masikuwo.
21 Ndipo pamenepo wina akati kwa inu, Onani Kristu ali pano; kapena, Onani, uko; musabvomereze;
22 pakuti adzauka Akristu onyenga ndi aneneri onyenga, ndipo adzacita zizindikilo ndi zozizwitsa, kuti akasoceretse, ngati nkutheka, osankhidwa omwe.
23 Koma yanganirani; onani ndakuuziranitu zinthu zonse, zisanafike.
24 Koma m'masikuwo, citatha cisautso cimeneco, dzuwa lidzadetsedwa, ndi mwezi sudzapatsa kuunika kwace,
25 ndi nyenyezi zidzagwa kucokera m'mwamba ndi mphamvu ziri m'mwamba zidzagwedezeka.
26 Ndipo pamenepo adzaona Mwana wa munthu alinkudza m'mitambo ndi mphamvu yaikuru, ndi ulemerero.
27 Ndipo pamenepo adzatuma angelo, nadzasonkhanitsa osankhidwa ace ocokera ku mphepo zinai, kuyambira ku malekezero ace a dziko lapansi, ndi kufikira ku malekezero a thambo.
28 Ndipo phunzirani ndi mkuyu fanizo lace; pamene pafika kuti nthambi yace ikhala yanthete, ndipo anaphuka masamba ace, muzindikira kuti layandikira dzinja;
29 comweco inunso, pamene muona zinthu izi zirikucitika, zindikirani kuti ali pafupi pakhomo.
30 Indetu ndinena ndi inu, Mbadwo uno sudzapita kufikira zinthu izi zonse zitacitika.
31 Thambo ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.
32 Koma za tsiku ilo, kapena nthawi yace sadziwa munthu, angakhale angelo m'Mwamba, angakhale Mwana, koma Atate ndiye.
33 Yang'anirani, dikirani, pempherani: pakuti simudziwa nthawi yace.
34 Monga ngati munthu wa paulendo, adacoka kunyumba kwace, nawapatsa akapolo ace ulamuliro, kwa munthu ali yense nchito yace, nalamulira wapakhomo adikire.
35 Cifukwa cace dikirani; pakuti simudziwa inu nthawi yace yakubwera mwini nyumba, kapena madzulo, kapena pakati pausiku, kapena pakulira tambala, kapena mamawa;
36 kuti angabwere balamantha nakakupezani muli m'tulo.
37 Ndipo cimene ndinena ndi inu ndinena kwa onse, Dikirani.
1 Ndipo popita masiku awiri kuli phwando la Paskha ndi mikate yopanda cotupitsa; ndipo ansembe akuru ndi alembi anafunafuna momcitira ciwembu, ndi kumupha:
2 pakuti anati, Paphwando ai, kuti pangakhale phokoso la anthu.
3 Ndipo pakukhala iye ku Betaniya m'nyumba ya Simoni wakhate, m'mene anaseama kudya, anadzapo mkazi ali nayo nsupa yaalabastero ya mafuta onunkhira bwino a nardo weni weni a mtengowapatali; naswa nsupayo, nawatsanulira pamutu pace.
4 Koma anakhalako ena anabvutika mtima mwa iwo okha, ndi kuti, Mafutawo atayidwa cifukwa ninji?
5 Pakuti mafuta amene akadagula marupiya atheka mazana atatu ndi mphambu zace, ndi kupatsa aumphawi. Ndipo anadandaulira mkaziyo.
6 Koma Yesu anati, Mlekeni, mumbvutiranji? wandicitira Ine nchito yabwino.
7 Pakuti muli nao aumphawi pamodzi ndi inu masiku onse, ndipo pali ponse pamene mukafuna mukhoza kuwacitira zabwino; koma Ine simuli nane masiku onse.
8 Iye wacita cimene wakhoza; anandidzozeratu thupi langa ku kuikidwa m'manda.
9 Ndipo ndithu ndinena ndi inu, Ponse pamene padzalalikidwa Uthenga Wabwino ku dziko lonse lapansi, icinso cimene anacita mkazi uyu cidzanenedwa, cikhale comkumbukira naco.
10 Ndipo Yudase Isikariote, ndiye mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anacoka napita kwa ansembe akuru, kuti akampereke Iye kwa iwo.
11 Ndipo pamene iwo anamva, anasekera, nalonjezana naye kuti adzampatsa ndalama. Ndipo iye anafunafuna pompereka Iye bwino.
12 Ndipo tsiku loyamba la mikate yopanda cotupitsa, pamene amapha Paskha, ophunzira ace ananena naye, Mufuna tinke kuti, tikakonze mkadyereko Paskha?
13 Ndipo anatuma awiri a ophunzira ace, nanena nao, Lowani m'mzinda, ndipo adzakomana nanu munthu wakusenza mtsuko wa madzi; mumtsate iye;
14 ndipo kumene akalowako iye, munene naye mwini nyumba, Mphunzitsi anena, Ciri kuti cipinda ca alendo canga, m'menemo ndikadye Paskha ndi ophunzira anga?
15 Ndipo iye yekha adzakusonyezani cipinda ca pamwamba cacikuru coyalamo ndi cokonzedwa; ndipo m'menemo mutikonzere.
16 Ndipo ophunzira anaturuka, nafika m'mzinda, napeza monga anati kwa iwo; ndipo anakonza Paskha.
17 Ndipo pofika madzulo anadza Iye pamodzi ndi khumi ndi awiriwo.
18 Ndipo pamene anaseama iwo kudya, Yesu anati, Ndithu ndinena ndi inu, Mmodzi wa inu adzandipereka Ine, ndiye wakudya ndi Ine pamodzi.
19 Anayamba iwo kukhala ndi cisoni, ndi kunena naye mmodzi mmodzi, kuti, Ndine kodi?
20 Ndipo anati kwa iwo, Mmodzi wa khumi ndi awiriwo, ndiye wakusunsa pamodzi ndi Ine m'mbale.
21 Pakuti Mwana wa munthu amukadi, monga kwalembedwa za Iye; koma tsoka munthuyo amene apereka Mwana wa munthu! Kukadakhala bwino kwa munthu ameneyo ngati sakadabadwa iye.
22 Ndipo pamene iwo analikudya, Iye anatenga mkate, ndipo pamene anadalitsa, ananyema, napereka kwa iwo, kuti, Tengani; thupi langa ndi ili.
23 Ndipo anatenga cikho, ndipo pamene adayamika, anapereka kwa iwo; ndipo iwo onse anamweramo.
24 Ndipo Iye anati kwa iwo, ici ndi mwazi wanga wa cipangano, wothiridwa cifukwa ca anthu ambiri.
25 Ndithu ndinena nanu, Sindidzamwanso cipatso ca mpesa, kufikira tsiku lijalo, limene ndidzamwa ico catsopano mu Ufumu wa Mulungu.
26 Ndipo atayimba nyimbo, anaturuka, namuka ku phiri la Azitona.
27 Ndipo Yesu ananena nao, Mudzakhumudwa nonsenu; pakuti kwalembedwa, Ndidzakantha mbusa, ndi nkhosa zidzamwazika.
28 Komatu nditadzauka ndidzatsogolera inu ku Galileya.
29 Koma Petro ananena naye, Angakhale adzakhumudwa onse, komatu ine iai.
30 Ndipo Yesu ananena naye, Ndithu ndinena ndi iwe, kuti lero, usiku uno, tambala asanalire kawiri, udzandikana Ine katatu.
31 Koma iye analimbitsa mau cilimbitsire, kuti, Ngakhale ndidzafa nanu, sindidzakana Inu. Ndipo onsewo anatero.
32 Ndipo iwo anadza ku malo dzina lace Getsemane; ndipo ananena kwa ophunzira ace, Bakhalani pano, kufikira ndikapemphera.
33 Ndipo anatenga pamodzi ndi Iye Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane, nayamba kudabwa kwambiri, ndi kusauka mtima ndithu.
34 Ndipo ananena nao, Moyo wanga uli wa cisoni cambiri, kufikira imfa. Bakhalani pano, nimudikire.
35 Ndipo Iye anapita m'tsogolo pang'ono, nagwa pansi, napemphera kuti ngati nkutheka nthawi imene impitirire.
36 Ndipo ananena, Abba, Atate, zinthu zonse zitheka ndi Inu; mundicotsere cikho ici; komatu si cimene ndifuna Ine, koma cimene mufuna Inu.
37 Ndipo anadza nawapeza iwo ali m'tulo, nanena ndi Petro, Simoni, ugona kodi? unalibe mphamvu yakudikira ora limodzi kodi?
38 Dikirani, pempherani, kuti mungalowe m'kuyesedwa; mzimutu uli wakufuna, koma thupi liri lolefuka.
39 Ndipo anacokanso, napemphera, nanena mau omwewo.
40 Ndipo anadzanso nawapeza ali m'tulo, pakuti maso ao analemeradi; ndipo sanadziwa comyankha Iye.
41 Ndipo anadza kacitatu, nanena nao, Gonani tsopano, nimupumule; cakwanira; yafika nthawi; onani Mwana wa munthu aperekedwa m'manja a anthu ocimwa.
42 Ukani, tizimuka; onani wakundiperekayo ali pafupi.
43 Ndipo pomwepo, Iye ali cilankhulire, anadza Yudase, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, ndipo pamodzi naye khamu la anthu, ali nao malupanga ndi mikunkhu, ocokera kwa ansembe akuru ndi alembi ndi akuru.
44 Ndipo wakumpereka Iye anawapatsa cizindikilo, nanena, Iye amene ndidzampsompsona, ndiyetu; mgwireni munke naye cisungire.
45 Ndipo atafika, pomwepo anadza kwa Iye, nanena, Rabi; nampsompsonetsa.
46 Ndipo anamthira manja, namgwira.
47 Koma mmodzi wina wa iwo akuimirirapo, anasolola lupanga lace, nakantha kapolo wace wa mkulu wa ansembe, namdula khutu lace.
48 Ndipo Yesu anayankha nati kwa iwo, Kodi mwaturuka ndi malupanga ndi mikunkhu kundigwira ine monga wacifwamba?
49 Masiku onse ndinali nanu m'Kacisi ndirikuphunzitsa, ndipo simunandigwira Ine; koma ici cacitika kuti malembo akwanitsidwe.
50 Ndipo iwo onse anamsiya Iye, nathawa.
51 Ndipo mnyamata wina anamtsata Iye, atapfundira pathupi bafuta yekha; ndipo anamgwira;
52 koma iye anasiya bafutayo, nathawa wamarisece.
53 Ndipo ananka naye Yesu kwa mkulu wa ansembe; ndipo anasonkhana kwa iye ansembe akuru onse ndi akuru a anthu, ndi alembi,
54 Ndipo Petro adamtsata Iye kutali, kufikira kulowa m'bwalo la mkulu wa ansembe; ndipo anali kukhala pansi pamodzi ndi anyamata, ndi kuotha moto.
55 Ndipo ansembe akuru ndi akuru a milandu onse anafunafuna umboni wakutsutsa nao Yesu kuti amuphe Iye; koma sanaupeza.
56 Pakuti ambiri anamcitira umboni wonama, ndipo umboni wao sunalingana.
57 Ndipo ananyamukapo ena, namcitira umboni wakunama, nanena kuti,
58 Ife tinamva Iye alikunena, kuti, Ine ndidzaononga Kacisi uyu wopangidwa ndi manja, ndi masiku atatu ndidzamanga wina wosapangidwa ndi manja.
59 Ndipo ngakhale momwemo umboni wao sunalingana.
60 Ndipo mkulu wa ansembe ananyamuka pakati, namfunsa Yesu, nanena, Suyankha kanthu kodi? Nciani ici cimene awa alikucitira mboni?
61 Koma anakhala cete, osayankhakanthu. Mkulu wa ansembe anamfunsanso, nanena naye, Kodi Iwe ndiwe Kristu, Mwana wace wa Wolemekezeka?
62 Ndipo Yesu anati, Ndine amene; ndipo mudzaona Mwana wa munthu alikukhala ku dzanja lamanja la mphamvu, ndi kudza ndi mitambo ya kumwamba.
63 Ndipo mkulu wa ansembe anang'amba maraya ace, nanena, Tifuniranjinso mboni zina?
64 Mwamva mwano wace; muyesa bwanji? Ndipo onse anamtsutsa Iye kuti ayenera kufa.
65 Ndipo ena mayamba kumthira malobvu Iye, adi kuphimba nkhope yace, ndi cumbwanyula, ndi kunena naye, Lota; ndipo anyamatawo ananpanda Iye kofu.
66 Ndipo pamene Petro anali iansi m'bwalo, anadzapo mmodzi va adzakazi a mkulu wa ansembe;
67 ndipo anaona Petro alikuotha noto, namyang'ana iye, nanena, wenso unali naye Mnazarene, Yesu.
68 Koma anakana, nanena, Sindidziwa kapena kumvetsa cimene ucinena iwe; ndipo anaturuka kunka kucipata; ndipo tambala analira.
69 Ndipo anamuona mdzakaziyo, nayambanso kunena ndi iwo akuimirirapo, Uyu ngwa awo.
70 Koma anakananso. Ndipo patapita kamphindi, akuimirirapo ananenanso ndi Petro, Zedi uli wa awo; pakutinso uti Mgalileya.
71 Koma iye anayamba kutemberera, ndi kulumbira, Sindimdziwa munthuyu mulikunena.
72 Ndipo pomwepo tambala analira kaciwiri. Ndipo Petro anakumbukila umo Yesu anati kwa iye, kuti, Tambala asanalire kawiri udzandikana katatu. Ndipo pakuganizira ici analira misozi.
1 Ndipo pomwepo mamawa anakhala upo ansembe akuru, ndi akuru a anthu, ndi alembi, ndi akuru a milandu onse, namanga Yesu, namtenga, nampereka kwa Pilato.
2 Ndipo Pilato anamfunsa Iye, Kodi ndiwe Mfumu ya Ayuda? Ndipo anayankha, nanena naye, Mwatero.
3 Ndipo ansembe akuru anamnenera Iye zinthu zambiri.
4 Ndipo Pilato anamfunsanso, nanena, Suyankha kanthu kodi? taona, akunenera Iwe zinthu zambiri zotere.
5 Koma Yesu sanayankhanso kanthu; kotero kuti Pilato anazizwa.
6 Ndipo adafuwamasulira paphwando wandende mmodzi, amene iwo anampempha,
7 Ndipo analipo wina dzina lace Baraba, womangidwa pamodzi ndi opanduka, amene anapha munthu mumphandumo.
8 Ndipo khamu la anthu anabwera nayamba kupempha kuti acite monga adafuwacitira.
9 Ndipo Pilato anawayankha, nanena nao, Kodi mufuna kuti ndikumasulireni Mfumu ya Ayuda?
10 Pakuti anazindikira kuti ansembe akuru anampereka Iye mwanjiru.
11 Koma ansembe akuru anasonkezera khamulo, kuti makamaka awamasulire Baraba.
12 Ndipo Pilato anawayankhanso, nati kwa iwo, Pamenepo ndidzacita ciani ndi Iye amene mumchula Mfumu ya Ayuda?
13 Ndipo anapfuulanso, Mpacikeni pamtanda.
14 Ndipo Pilato ananena nao, Pakuti Iye anacita coipa cotani? Koma iwo anapfuulitsatu, Mpacikeni Iye.
15 Ndipo Pilato pofuna kuwakhazika mtima anthuwo, anawamasulira Baraba, napereka Yesu, atamkwapula, akampacike pamtanda.
16 Ndipo asilikari anacoka naye nalowa m'bwalo, ndilo Pretorio; nasonkhanitsa gulu lao lonse.
17 Ndipo anambveka Iye cibakuwa, naluka korona waminga, nambveka pa Iye;
18 ndipo anayamba kumlankhula Iye, kuti, Tikuoneni, Mfumu ya Ayuda!
19 Ndipo anampanda Iye pamutu pace ndi bango, namthira malobvu, nampindira maondo, namlambira.
20 Ndipo atatha kumnyoza anambvula cibakuwaco nambveka Iye zobvala zace. Ndipo anaturuka naye kuti akampacike Iye pamtanda.
21 Ndipo anakangamiza wina wopitirirapo, Simoni wa ku Kurene, alikucokera kuminda, atate wao wa Alesandere ndi Rufu, kuti anyamule mtanda wace.
22 Ndipo anamtenga kunka naye ku malo Golgota, ndiwo, osandulika, Malo-a-bade.
23 Ndipo anampatsa vinyo wosanganiza ndi mure; koma Iye sanamlandira.
24 Ndipo anampacika Iye, nagawana zobvala zace mwa iwo okha, ndi kucita maere pa izo, kuti adziwe yense adzatengaciani.
25 Ndipo panali ora lacitatu, ndipo anampacika Iye.
26 Ndipo lembo la mlandu wace linalembedwa pamwamba, MFUMU YAAYUDA.
27 Ndipo anapacika pamodzi ndi Iye acifwamba awiri; mmodzi ku dzanja lace lamanja ndi wina kulamanzere.[
28 ]
29 Ndipo iwo akupitirirapo anamcitira mwano, napukusa mitu yao, nanena, Ha! iwe wakupasula Kacisi, ndi kummanga masiku atatu,
30 udzipulumutse mwini, nutsike pamtanda.
31 Moteronso ansembe akuru anamtonza mwa iwo okha pamodzi ndi alembi, nanena, Anapulumutsa ena; sakhoza kudzipulumutsa yekha.
32 Atsike tsopano pamtanda, Kristu Mfumu ya Israyeli, kuti tione, ndi kukhulupirira. Ndipo iwo akupacikidwa naye anamlalatira.
33 Ndipo pofika ora lacisanu ndi cimodzi, panali mdima pa dziko lonse, kufikira ora lacisanu ndi cinai.
34 Ndipo pa ora lacisanu ndi cinai Yesu anapfuula ndi mau okweza, Eloi, Eloi, lama sabakitani? ndiko kusandulika, Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji Ine?
35 Ndipo ena akuimirirapo, paku mva, ananena, Taonani, aitana Eliya
36 Ndipo anathamanga wina, nadzaza cinkhupule ndi vinyo wosasa naciika pabango, namwetsa Iye nanena, Lekani; tione ngati Eliys adza kudzamtsitsa.
37 Ndipo Yesr anaturutsa mau okweza, napereka mzimu wace.
38 Ndipo cinsart cocinga ca m'Kacisi cinang'ambika pakati, kuyambira kumwamba kufikira pansi.
39 Ndipo pamene kenturiyo, woimirirapo popenyana ndi Iye, anaona kuti anapereka mzimu kotero, anati, Zoonadi, munthu uyu anali Mwana wa Mulungu.
40 Ndipo analinso kumeneko akazi akuyang'anira kutali; mwa iwo anali Maliya wa Magadala, ndi Maliya amace wa Yakobo wamng'ono ndi wa Yose, ndi Salome;
41 amene anamtsata Iye, pamene anali m'Galileya, namtumikira; ndi akazi ena ambiri, amene anakwera kudza ndi Iye ku Yerusalemu.
42 Ndipo atafika tsono madzulo, popeza mpa tsiku lokonzera, ndilo la pambuyo pa Sabata,
43 anadzapo Y osefe wa ku Arimateya, mkulu wa mirandu womveka, amene yekha analikuyembekezera Ufumu wa Mulungu; nalimba mtima nalowa kwa Pilato, napempha mtembo wace wa Yesu.
44 Ndipo Pilato anazizwa ngati adamwaliradi; naitana kenturiyo, namfunsa ngati adamwalira kale.
45 Ndipo pamene anacidziwa ndi kenturiyo, anamninkha Yosefe ntembowo.
46 Ndipo anagula oafuta, namtsitsa Iye, namkulunga n'bafutamo, namuika m'manda osenedwa m'thanthwe; nakunkhunicira mwala pa khomo la manda.
47 Ndipo Maliya wa Magadala ndi Maliya amace wa Yose anapenya pomwe anaikidwapo.
1 Ndipo litapita Sabata, Maliya wa Magadala, ndi Maliya amace wa Yakobo, ndi Salome, anagula zonunkhira, kuti akadze kumdzoza Iye.
2 Ndipo anadza kumanda mamawa tsiku loyamba la Sabata, litaturuka dzuwa.
3 Ndipo analikunena mwa okha, Adzatikunkhunizira ndam mwalawo, pa khomo la manda?
4 Ndipo pamene anakweza maso anaona kuti mwala wakunkhunizidwa pakuti unali waukuru ndithu.
5 Ndipo pamene analowa m'manda, anaona mnyamata alikukhala ku mba li va ku dzanja lamanja, wobvala mwinjiro woyera; ndipo iwo anadabwa.
6 Ndipo iye ananena nao, Musadabwe: mulikufuna Yesu Mnazarene amene anapacikidwa: anauka; sali pano; taonani, mbuto m'men e anaikamo Iye!
7 Koma mukani, uzani ophunzira ace, ndi Petro, kuti akutsogolerani inu ku Galileya; kumeneko mudzamuona Iye, monga ananena ndi inu.
8 Ndipo anaturuka iwo, nathawa kumanda; pakuti kunthunthumira ndi kudabwa kwakukuru kudawagwira; ndipo sanauza kanthu kwa munthu ali yense; pakuti anacitamantha.
9 Ndipo pamene Iye adauka mamawa tsiku loyamba la sabata, anayamba kuonekera kwa Maliya wa Magadala, amene Iye adamturutsira ziwanda zisanu ndi ziwiri.
10 Iyeyu anapita kuwauza iwo amene adafokhala naye, ali ndi cisoni ndi kulira misozi.
11 Ndipo iwowo, pamene anamva kuti ali moyo, ndi kuti adapenyeka kwa iye, sanamvera.
12 Ndipo zitatha izi, anaonekanso Iye m'maonekedwe ena kwa awiri a iwo alikuyenda kupita kumiraga,
13 Ndipo iwowa anacoka nawauza otsala; koma iwo omwe sanawabvomereza.
14 Ndipo citatha ico anaonekera kwa khumi ndi mmodzi iwo okha, alikuseama pacakudya; ndipo anawadzudzula cifukwa ca kusabvomereza kwao ndi kuuma mtima, popeza sanabvomereza iwo amene adamuona, atauka Iye.
15 Ndipo ananena nao, mukani ku dziko lonse lapansi, lalikirani Uthenga Wabwino kwa olengedwa onse.
16 Amene akhulupirira nabatizidwa, adzapulumutsidwa; koma amene sakhulupirira adzalangidwa.
17 Ndipo zizindikilo izi zidzawatsata iwo akukhulupirira; m'dzina langa adzaturutsa ziwanda; adzalankhula ndi malankhulidwe atsopano;
18 adzatola njoka, ndipo ngakhale akamwa kanthu kakufa nako, sikadzawapweteka; adzaika manja ao pa odwala, ndipo adzacira.
19 Pamenepo Ambuye Yesu, ata-tha kulankhula nao, analandiridwa Kumwamba, nakhala pa dzanja lamanja la Mulungu.
20 Ndipo iwowa anaturuka, nalalikira ponse ponse, ndipo Ambuye anacita nao pamodzi, natsimikiza mau ndi zizindikilo zakutsatapo, Amen.