1

1 BUKU la kubadwa kwa Yesu Kristu, mwana wa Davide, mwana wa Abrahamu.

2 Abrahamu anabala Isake; ndi Isake anabala Yakobo; ndi Yakobo anabala Yuda ndi abale ace;

3 ndi Yuda anabala Farese ndi Zara mwa Tamare; ndi Farese anabala Ezronu; ndi Ezronu anabala Aramu;

4 ndi Aramu anabala Aminadabu; ndi Aminadabu anabala Naasoni; ndi Naasoni anabala Salimoni;

5 ndi Salimoni anabala Boazi mwa Rahabe; ndi Boazi anabala Obede mwa Rute; ndi Obede anabala Jese;

6 ndi Jese anabala Davide mfumuyo. Ndipo Davide anabala Solomo mwa mkazi wa Uriya;

7 ndi Solomo anabala Rehabiamu; ndi Rehabiamu anabala Abiya; ndi Abiya anabala Asa;

8 ndi Asa anabala Yosafate; ndi Yosafate anabala Yoramu; ndi Yoramu anabala Uziya;

9 ndi Uziya anabala Yotamu; ndi Yotamu anabala Ahazi; ndi Ahazi anabala Hezekiya;

10 ndi Hezekiya anabala Manase; ndi Manase anabala Amoni; ndi Amoni anabala Yosiya;

11 ndi Yosiya anabala Yekoniya ndi abale ace pa nthawi yakutengedwa kunka ku Babulo.

12 Ndipo pambuyo pace pa kutengedwako ku Babulo, Yekoniya anabala Salatieli; ndi Saiatieli anabala Zerubabele;

13 ndi Zerubabele anabala Abiyudi; ndi Abiyudi anabala Eliyakimu; ndi Eliyakimu anabala Azoro;

14 ndi Azoro anabala Sadoki; ndi Sadoki anabala Akimu; ndi Akimu anabala Eliyudi;

15 ndi Eliyudi anabala Eleazara; ndi Eleazara anabala Matani; ndi Matani anabala Yakobo;

16 ndi Yakobo anabala Yosefe, mwamuna wace wa Mariya, amene Yesu, wochedwa Kristu, anabadwa mwa iye.

17 Motero mibadwo yonse kuyambira pa Abrahamu kufikira kwa Davide ndiyo mibadwo khumi ndi inai; ndi kuyambira pa Davide kufikira pa kutengedwa kunka ku Babulo mibadwo khumi ndi inai; ndi kuyambira pa kutengedwa kunka ku Babulo kufikira kwa Kristu mibadwo khumi ndi inai.

18 Ndipo kubadwa kwace kwa Yesu Kristu kunali kotere: Amai wace Mariya anapalidwa ubwenzi ndi Yosefe, koma asanakomane iwowo, anapezedwa iye ali ndi pakati mwa Mzimu Woyera.

19 Koma Yosefe, mwamuna wace, anali wolungama, ndiponso sanafuna kunyazitsa iye, nayesa m'mtima kumleka iye m'tseri,

20 Koma pakusinkhasinkha iye zinthu izi, onani, mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye m'kulota, nanena, Yosefe, mwana wa Davide, usaope kudzitengera wekha Mariya mkazi wako; pakuti ico colandiridwa mwa iye ciri ca Mzimu Woyera.

21 Ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo udzamucha dzina lace Yesu; pakuti Iyeyo adzapulumutsa anthu ace ku macimo ao.

22 Ndipo zonsezi zinakhala kuti cikacitidwe conenedwa ndi Ambuye mwa mneneri, ndi kuti,

23 Onani namwali adzaima, Nadzabala mwana wamwamuna, Ndipo adzamucha dzina lace, Emanueli; ndilo losandulika, Mulungu nafe.

24 Ndipo Yosefe anauka tulo tace, nacita monga anamuuza mngelo wa Ambuye, nadzitengera yekha mkazi wace;

25 ndipo sanamdziwa iye kufikira atabala rriwana wace; namucha dzina lace Yesu.

2

1 Ndipo pa kubadwa kwace kwa Yesu m'Betelehemu wa Yudeya m'masiku a Herode mfumu, onani, Anzeru a kum'mawa anafika ku Yerusalemu,

2 nati, Ali kuti amene anabadwa Mfumu ya Ayuda? cifukwa tinaona nyenyezi yace kum'mawa, ndipo tinadzera kudzamlambira Iye.

3 Ndipo Herode mfumuyo pakumva ici anabvutika, ndi Yerusalemu yense pamodzi naye.

4 Ndipo pamene anasonkhanitsa ansembe akuru onse ndi alembi a anthu, anafunsira iwo, Adzabadwira kuti Kristuyo?

5 Ndipo anamuuza iye, M'Betelehemu wa Yudeya; cifukwa kunalembedwa kotere ndi mneneri, kuti,

6 Ndipo iwe: Betelehemu, dziko la Yudeya, Sukhala konse wamng'onong'ono mwa akuru a Yudeya. Pakuti Wotsogolera adzacokera mwaiwe, Amene adzaweta anthu anga Aisrayeli.

7 Pomwepo Herode anawaitana Anzeruwo m'tseri, nafunsitsa iwo nthawi yace idaoneka nyenyeziyo.

8 Nawatumiza ku Betelehemu, nati, Yendani mufunitsitse za kamwanako; ndipo pamene mudzampeza, mundibwezere mau, kuti inenso ndidzadze kudzamlambira Iye.

9 Ndipo iwo, m'mene anamva mfumu, anamuka; ndipo onani, nyenyezi ija anaiona kum'mawa, inawatsogolera iwo, kufikira inadza niima pamwamba pomwe panali kamwanako.

10 Ndipo iwo poona nyenyeziyo, anakondwera ndi kukondwera kwakukuru.

11 Ndipo pofika ku nyumba anaona kamwanako ndi Mariya amace, ndipo anagwa pansi namgwadira Iye; namasula cuma cao, nampatsa Iye mitulo, ndiyo golidi ndi libano ndi mure.

12 Ndipo iwo, pocenjezedwa m'kulota kuti asabwerere kwa Herode, anacoka kupita ku dziko lao pa njira yina.

13 Ndipo pamene iwo anacoka, onani, mngelo wa Ambuye anaonekera kwa Yosefe m'kulota, nati, Tauka, nutenge kamwanako ndi amace, nuthawire ku Aigupto, nukakhale kumeneko kufikira ndidzakuuza iwe; pakuti Herode adzafuna kamwana kukaononga Iko.

14 Ndipo iye ananyamuka natenga kamwana ndi amace usiku, nacoka kupita ku Aigupto;

15 nakhalabe kumeneko kufikira atamwalira Herode; kuti cikacitidwe conenedwa ndi Ambuye mwa mneneri kuti, Ndinaitana Mwana wanga aturuke m'Aigupto.

16 Pamenepo Herode, poona kuti anampusitsa Anzeruwo, anapsa mtima ndithu, natumiza ena kukaononga tiana tonse ta m'Betelehemu ndi ta m'miraga yace yonse, takufikira zaka ziwiri ndi tating'ono tonse, monga mwa nthawi imeneyo iye anafunsitsa kwa Anzeruwo.

17 Pomwepo cinacitidwa conenedwa ndi Yeremiya mneneri, kuti,

18 Mau anamveka m'Rama, Maliro ndi kucema kwambiri; Rakele wolira ana ace, Wosafuna kusangalatsidwa, Cifukwa palibe iwo.

19 Koma pakumwalira Herode, onani, mngelo wa Ambuye anaonekera m'kulota kwa Yosefe m'Aigupto,

20 nati, Tauka, nutenge kamwana ndi amace, nupite ku dziko la Israyeli: cifukwa anafa uja wofuna moyo wace wa kamwanako.

21 Ndipo anauka iye, natenga kamwana ndi amace, nalowa m'dziko la Israyeli.

22 Koma pakumva iye kuti Arikelao anali mfumu ya Yudeya m'malo mwa atate wace Herode, anacita mantha kupita kumeneko; ndipo pamene anacenjezedwa ndi Mulungu m'kulota, anamuka nalowa ku dziko la Galileya,

23 nadza nakhazikika m'mudzi dzina lace Nazarete kuti cikacitidwe conenedwa ndi aneneri kuti, Adzachedwa Mnazarayo.

3

1 Ndipo masiku aja anadza Yohane Mbatizi, nalalikira m'cipululu ca Yudeya,

2 nanena, Tembenukani mitima; cifukwa Ufumu wa Kumwamba wayandikira.

3 Pakuti uyu ndiye ananenayo Yesaya mneneri, kuti, Mau a wopfuula m'cipululu, Konzani khwalala la Ambuye, Lungamitsani njira zace.

4 Ndipo Yohane yekhayo anali naco cobvala cace ca ubweya wangamila, ndi lamba lacikopa m'cuuno mwace; ndi cakudya cace cinali dzombe ndi uci wa kuthengo.

5 Pamenepo panamturukira iye ku Yerusalemu, ndi Yudeya lonse, ndi dziko lonse loyandikana ndi Yordano;

6 nabatizidwa ndi iye mu mtsinjewo wa Yordano, alikuulula macimo ao.

7 Ndipo iye pakuona ambiri a Afarisi ndi a Asaduki akudza ku ubatizo wace, anati kwa iwo, Obadwa a njoka inu, ndani anakulangizani kuthawa mkwiyo ulinkudza?

8 Onetsani inu zipatso zakuyenera kutembenuka mtima:

9 ndipo musamayesa kunena mwa inu nokha, Atate wathu tiri naye Abrahamu; pakuti ndinena kwa inu kuti mwa miyala iyi Mulungu akhoza kuukitsira Abrahamu ana.

10 Ndiponso tsopano lino nkhwangwa yaikidwa pa mizu ya mitengo; cifukwa cace mtengo uli wonse wosabala zipatso zabwino udulidwa nuponyedwa pamoto,

11 Inetu ndikubatizani inu ndi madzi kuloza ku kutembenuka mtima; koma Iye wakudza pambuyo panga, ali wakundiposa mphamvu, amene sindiyenera kunyamula nsapato zace: Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto:

12 couluzira cace ciri m'dzanja lace, ndipo adzayeretsa padwale pace; ndipo adzasonkhanitsa tirigu wace m'ciruli, koma mankhusu adzatentha ndi moto wosazima.

13 Pamenepo Yesu anacokera ku Galileya nadza ku Yordano kwa Yohane, kudzabatizidwa ndi iye.

14 Koma Yohane anati amkanize, nanena, Ndiyenera ine kubatizidwa ndi Inu, ndipo Inu mudza kwa ine kodi?

15 Koma Yesu anayankha, nati kwa iye, Balola tsopano: pakuti kuyenera ife kukwaniritsa cilungamo conse motero. Pamenepo anamlola Iye.

16 Ndipo Yesu, pamene anabatizidwa, pomwepo anaturuka m'madzi: ndipo onani, miyamba inamtsegukira Iye, ndipo anapenya Mzimu wa Mulungu wakutsika ngati nkhunda nudza nutera pa Iye;

17 ndipo onani, mau akucokera kumiyamba akuti, Uyu ndiye Mwana wanga wokondedwa, mwa Iyeyu ndikondwera.

4

1 Pamenepo Yesu anatengedwa ndi Mzimu kumka kucipululu kukayesedwa ndi mdierekezi.

2 Ndipo pamene Iye analibe kudya masiku makumi anai usana ndi usiku, pambuyo pace anamva njala.

3 Ndipo woyesayo anafika nanena kwa Iye, Ngati muli Mwana wa Mulungu, tauzani kuti miyala iyi isanduke mikate.

4 Koma Iye anayankha nati, Kwalembedwa, Munthu sadzakhala ndi moyo ndi mkate wokha, koma ndi mau onse akuturuka m'kamwa mwa Mulungu.

5 Pamenepo mdierekezi anamuka naye ku mzinda woyera; namuika Iye pamwamba pa cimbudzi ca Kacisi,

6 nanena naye, Ngati muli Mwana wa Mulungu, mudzigwetse nokha pansi: pakuti kwalembedwa, kuti, Adzauza angelo ace za iwe, Ndipo pa manja ao adzakunyamulaiwe, Ungagunde konse phazi lako pamwala.

7 Yesu ananena naye, Ndiponso kwalembedwa, Usamuyese Ambuye Mulungu wako.

8 Pomwenso mdierekezi anamuka naye ku phiri lalitari, namuonetsa maiko onse a dziko lapansi, ndi ulemerero wao;

9 nati kwa Iye, Zonse ndikupatsani Inu, ngati mudzagwa pansi ndi kundigwadira ine.

10 Pomwepo Yesu ananena kwa iye, Coka Satana, pakuti kwalembedwa, Ambuye Mulungu wako udzamgwadira, Ndipo Iye yekha yekha udzamlambira.

11 Pomwepo mdierekezi anamsiya Iye, ndipo onani, angelo anadza, namtumikira Iye.

12 Ndipo pamene Yesu anamva kuti anampereka Yohane, anamuka kulowa ku Galileya;

13 ndipo anacoka ku Nazarete nadza nakhalitsa Iye m'Kapernao ira pambali pa nyanja, m'malire a Zebuloni ndi Nafitali:

14 kuti cikacitidwe conenedwa ndi Yesaya mneneri, kuti,

15 It Dziko la Zebuloni ndi dziko la N afitali, Njira ya kunyanja, kutsidya lija la Yordano, Galileya la anthu akunja,

16 Anthu akukhala mumdima Adaona kuwala kwakukuru, Ndi kwa iwo okhala m'malo mthunzi wa imfa, Kuwala kunaturukira iwo.

17 Kuyambira pamenepo Yesu anayamba kulalikira, ndi kunena, Tembenukani mitima, pakuti Ufumu wa Kumwamba wayandikira.

18 Ndipo pamene Yesu analikuyenda m'mbali mwa nyanja ya Galileya, anaona abale awiri, Simoni wonenedwa Petro, ndi Andreya, mbale wace, analikuponya psasa m'nyanja; popeza anali asodzi a nsomba.

19 Ndipo Iye ananena nao, Tiyeni pambuyo panga, ndidzakusandutsani asodzi a anthu.

20 Ndipo iwo anasiya pomwepo makokawo, namtsata Iye.

21 Ndipo popitirirapo Iye anaona abale ena awiri, Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi Yohane mbale wace, m'ngalawa, pamodzi ndi Zebedayo atate wao, analikusoka makoka ao; ndipo anaitana iwo.

22 Ndipo anasiya pomwepo ngalawayo ndi atate wao, namtsata Iye.

23 Ndipo Yesu anayendayenda m'Galileya monse, analikuphunzitsa m'masunagoge mwao, nalalikira uthenga wabwino wa Ufumu, naciritsa nthenda zonse ndi kudwala konse mwa anthu.

24 Ndipo mbiri yace inabuka ku Suriya konse: ndipo anatengera kwa Iye onse akudwala, ogwidwa ndi nthenda ndi mazunzo a mitundu mitundu, ndi ogwidwa ndi mizimu yoipa, ndi akhunyu, ndi amanjenje; ndipo Iye anawaciritsa.

25 Ndipo inamtsata mipingo mipingo ya anthu ocokera ku Galileya, ndi ku Dekapole ndi ku Yerusalemu, ndi ku Yudeya, ndi ku tsidya lija la Yordano.

5

1 Ndipo m'mene Iye anaona makamu, anakwera m'phiri; ndipo m'mene Iye anakhala pansi, anadza kwa Iye ophunzira ace;

2 ndipo anatsegula pakamwa, nawaphunzitsa iwo, nati:

3 Odala ali osauka mumzimu; cifukwa uli wao Ufumu wa Kumwamba.

4 Odala ali acisoni; cifukwa adzasangalatsidwa.

5 Odala ali akufatsa; cifukwa adzalandira dziko lapansi.

6 Odala ali akumva njala ndi ludzu la cilungamo; cifukwa adzakhuta.

7 Odala ali akucitira cifundo; cifukwa adzalandira cifundo.

8 Odala ali oyera mtima; cifukwa adzaona Mulungu.

9 Odala ali akucita mtendere; cifukwa adzachedwa ana a Mulungu.

10 Odalaaliakuzunzidwacifukwa ca cilungamo: cifukwa uli wao Ufumu wa Kumwamba.

11 Odala muli inu m'mene adzanyazitsa inu, nadzazunza inu, nadzakunenerani monama zoipa ziri zonse cifukwa ca Ine.

12 Sekerani, sangalalani: cifukwa mphotho yanu ndi yaikuru m'Mwamba: pakuti potero anazunza aneneri anakhalawo musanabadwe inu.

13 Inu ndinu mcere wa dziko lapansi; koma mcerewo ngati uka: sukuluka, adzaukoleretsa ndi ciani? Pamenepo sungakwanirenso kanthu konse, koma kuti ukaponyedwe kunja, nupondedwe ndi anthu.

14 Inu ndinu kuunika kwa dziko lapansi. Mudzi wokhazikika pamwamba pa phiri sungathe kubisika.

15 Kapena sayatsa nyali, ndi kuibvundikira m'mbiya, koma aiika iyo pa coikapo cace; ndipo iunikira onse: ali m'nyumbamo.

16 Comweco muwalitse inu kuunika kwanu pamaso pa anthu, kuti pakuona nchito zanu zabwino, alemekeze Atate wanu wa Kumwamba.

17 Musaganize kuti ndinadza Ine kudzapasula cilamulo kapena ane, neri: sindinadza kupasula, koma kukwaniritsa.

18 Pakuti indetu ndinena kwa inu, Kufikira litapitirira thambo ndi dziko, kalemba kakang'ono kamodzi kapena kansonga kace kamodzi sikadzaeokera kucilamulo, kufikira zitacitidwa zonse.

19 Cifukwa cace yense wakumasula limodzi la malangizo amenewa ang'onong'ono, nadzaphunzitsa anthu comweco, adzachulidwa wamng'onong'ono mu Ufumu wa Kumwamba; koma yense wakucita ndi kuphunzitsa awa, iyeyu adzachulidwa wamkuru mu Ufumu wa Kumwamba.

20 Pakuti ndinena ndi inu, ngati cilungamo canu sicicuruka coposa ca alembi ndi Afarisi, simudzalowa konse mu Ufumu wa Kumwamba.

21 Munamva kuti kunanenedwa kwa iwo akale, Usaphe; koma yense wakupha adzakhala wopalamula mlandu:

22 koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wokwiyira mbale wace wopanda cifukwa adzakhala wopalamula mlandu; ndipo amene adzanena ndi mbale wace, Wopanda pace iwe, adzakhala wopalamula mlandu wa akuru: koma amene adzati, Citsiru iwe: adzakhala wopalamula gehena wamoto.

23 Cifukwa cace ngati ulikupereka mtulo wako pa guwa la nsembe, ndipo pomwepo ukakumbukira kuti mbale wako ali ndi kanthu pa iwe,

24 usiye pomwepo mtulo wako kuguwako, nucoke, nuyambe kuyanjana ndi mbale wako, ndipo pamenepo idza nupereke mtulo wako.

25 Fulumira kuyanjana ndi mnzako wamlandu, pamene uli naye panjira; kapena mnzako wamlandu angakupereke iwe kwa woweruza mlandu, ndi woweruzayo angapereke iwe kwa msilikari, nuponyedwe iwe m'nyumba yandende.

26 Indetu ndinena ndi iwe, sudzaturukamo konse, koma utalipa kakobiri kakumariza ndiko.

27 Munamva kuti kunanenedwa, Usacite cigololo;

28 koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wakuyang'ana mkazi kumkhumba, pamenepo watha kucita naye cigololo mumtima mwace.

29 Koma 1 ngati diso lake lamanja likulakwitsa iwe, ulikolowole, nulitaye; pakuti nkwabwino kwa iwe, kuti cimodzi ca ziwalo zako cionongeke, losaponyedwa thupi lako lonse m'gehena.

30 Ndipo 2 ngati dzanja lako lamanja likulakwitsa iwe, ulidule, nulitaye; pakuti nkwabwino kwa iwe kuti cimodzi ca ziwalo zako cionongeke, losamuka thupi lako lonse kugehena.

31 Kunanenedwanso, Yense wakucotsa mkazi wace 3 ampatse iye cilekaniro:

32 koma Ine ndinena kwa inu, kuti 4 yense wakucotsa mkazi wace, kosati cifukwa ca cigololo, amcititsa cigololo: ndipo amene adzakwata wocotsedwayo acita cigololo.

33 Ndiponso, munamva kuti kunanenedwa kwa iwo akale, 5 Usalumbire konama, koma udzapereka kwa Ambuye zolumbira zako:

34 koma Ine ndinena kwa inu, 6 Musalumbire konse, kapena kuchula Kumwamba, cifukwa kuli cimpando ca Mulungu;

35 7 kapena kuchula dziko lapansi, cifukwa liri popondapo mapazi ace; kapena kuchula Yerusalemu, cifukwa kuli mzinda wa Mfumu yaikurukuru.

36 8 Kapena usalumbire ku mutu wako, cifukwa sungathe kuliyeretsa mbu kapena kulidetsa bii tsitsi limodzi.

37 9 Kama manenedwe anu akhale, Inde, inde; Iai, iai; ndipo coonjezedwa pa izo cicokera kwa woipayo.

38 Munamva kuti kunanenedwa, 10 Diso kulipa diso, ndi dzino kulipa dzino:

39 koma ndinena kwa inu, 11 Musakanize munthu woipa; koma amene adzakupanda iwe pa tsaya lako Lamanja, umtembenuzire linanso.

40 Ndipo kwa iye wofuna kupita nawe kumlandu ndi kutenga malaya ako, umlolezenso copfunda cako.

41 Ndipo 12 amene akakukakamiza kumperekeza njira imodzi, upite naye ziwiri.

42 Kwa iye wopempha iwe umpatse, ndipo kwa iye 13 wofuna kukukongola usampotolokere.

43 Munamva kuti kunanenedwa, 14 Uzikondana ndi mnansi wako, ndi kumuda mdani wako:

44 koma Ine ndinena kwa inu, 15 Kondanani nao adani anu, ndi 16 kupempherera iwo akuzunza inu;

45 kotero kuti mukakhale ana a Atate wanu wa Kumwamba; cifukwa Iye amakwezera dzuwa lace pa oipa ndi pa abwino, namabvumbitsira mvula pa olungama ndi pa osalungama.

46 Cifukwa kuti 17 ngati muwakonda akukondana ndi inu mphotho yanji muli nayo? kodi angakhale amisonkho sacita comweco?

47 Ndipo ngati mulankhula abale anu okha okha, mucitanji coposa ena? Kodi angakhale anthu akunja sacita comweco?

48 Cifukwa cace inu 18 mukhale angwiro, monga Atate wanu wa Kumwamba ali wangwiro.

6

1 Yang'anirani kuti musacite zolungama zanu pamaso pa anthu kuti muonekere kwa iwo; pakuti ngati mutero mulibe mphotho ndi Atate wanu wa Kumwamba.

2 Cifukwa cace pamene pali ponse upatsa mphatso zacifundo, usamaomba lipenga patsogolo pako, monga amacita onyenga m'masunagoge, ndi m'makwalala, kotero kuti atamandidwe ndi anthu. Indetu ndinena kwa inu, Iwo alandiriratu mphotho zao.

3 Koma iwe popatsa mphatso zacifundo, dzanja lako lamanzere lisadziwe cimene licita dzanja lako lamanja;

4 kotero kuti mphatso zako zacifundo zikhale zam'tseri; ndipo Atate wako wakuona m'tseri adzakubwezera iwe.

5 Ndipo pamene mupemphera, musakhale monga onyengawo; cifukwa iwo akonda kuimirira ndi kupemphera m'masunagoge, ndi pa mphambano za makwalala, kuti aonekere kwa anthu. Indetu ndinena kwa inu, Iwo alandiriratu mphotho zao.

6 Koma iwe popemphera, Iowa m'cipinda cako, nutseke citseko cako, nupemphere Atate wako ali m'tseri, ndipo Atate wako wakuona m'tseri adzakubwezera iwe.

7 Ndipo popemphera musabwereze-bwereze cabe iai, monga amacita anthu akunja, cifukwa ayesa kuti adzamvedwa ndi kulankhula-lankhula kwao.

8 Cifukwa cace inu musafanane nao: pakuti Atate wanu adziwa zomwe muzisowa, inu musanayambe kupempha Iye.

9 Cifukwa cace pempherani inu comweci: Atate wathu wa Kumwamba, Dzina lanu liyeretsedwe.

10 Ufumu wanu udze. Kufuna kwanu kucitidwe, monga Kumwamba comweco pansi pano.

11 Mutipatse ife lero cakudya cathu calero.

12 Ndipo mutikhululukire mangawa athu, monga ifenso takhululukira amangawa anthu.

13 Ndipo musatitengere kokatiyesa, koma mutipulumutse kwa woipayo.

14 Pakuti ngati mukhululukira anthu zolakwa zao adzakhululukira inunso Atate wanu wa Kumwamba.

15 Koma ngati simukhululukira anthu zolakwa zao, Atate wanunso sadzakhululukira zolakwa zanu.

16 Ndipo pamene ponse musala kudya, musakhale ndi nkhope yacisoni, ngati onyengawo; pakuti aipitsa nkhope zao, kuti aonekere kwa anthu kuti alimkusala kudya. Indetu ndinena kwa inu, Iwo alandiriratu mphotho zao.

17 Koma iwe, posala kudya, dzola mutu wako, ndi kusamba nkhope yako:

18 kuti usaonekere kwa anthu kuti ulikusala kudya, koma kwa Atate wako ali m'tseri: ndipo Atate wako wakuona m'tseri adzakubwezera iwe.

19 Musadzikundikire nokha cuma pa dziko lapansi, pamene njenjete ndi dzimbiri ziononga; ndi pamene mbala ziboola ndi kuba:

20 koma mudzikundikire nokha cuma m'Mwamba, pamene njenjete kapena dzimbiri siziononga, ndipo mbala siziboola ndi kuba;

21 pakuti kumene kuli cuma cako, komwe udzakhala mtima wakonso.

22 Diso ndilo nyali ya thupi; cifukwa cace ngati diso lako liri la kumodzi, thupi lako lonse lidzakhala lowalitsidwa.

23 Koma ngati diso lako liri loipa, thupi lako lonse lidzakhala lodetsedwa. Cifukwa cace ngati kuwala kumene kuli mwa inu kuli mdima, mdimawo ndi waukuru ndithu!

24 Palibe munthu angathe kukhala kapolo wa ambuye awiri: pakuti pena adzamuda mmodziyo, ndi kukonda winayo; pena adzakangamira kwa mmodzi, nadzanyoza wina. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa Cuma.

25 Cifukwa cace ndinena kwa inu, Musadere nkhawa moyo wanu, cimene mudzadya ndi cimene mudzamwa; kapena thupi lanu, cimene mudzabvala. Kodi moyo suli woposa cakudya, ndi thupi loposa cobvala?

26 Yang'anirani mbalame za kumwamba, kuti sizimafesa ai, kapena sizimatema ai, kapena sizimatutira m'nkhokwe; ndipo Atate wanu wa Kumwamba azidyetsa. Nanga inu mulibe kusiyana nazo kuziposa kodi?

27 Ndipo ndani wa inu ndi kudera nkhawa angathe kuonjezera pa msinkhu wace mkono umodzi?

28 Ndipo muderanji nkhawa ndi cobvala? Tapenyetsani maluwa a kuthengo, makulidwe ao; sagwiritsa nchito, kapena sapota:

29 koma ndinena kwa inu, kuti angakhale Solomo mu ulemerero wace wonse sanabvala monga limodzi la amenewa.

30 Koma ngati Mulungu abveka cotero maudzu a kuthengo, akhala lero, ndi mawa oponyedwa pamoto, nanga si inu kopambana ndithu, inu akukhulupirira pang'ono?

31 Cifukwa cace musadere nkhawa, ndi kuti, Tidzadya ciani? kapena, Tidzamwa ciani? kapena, Tidzabvala ciani?

32 Pakuti anthu akunja azifunitsa zonse zimenezo; pakuti Atate wanu wa Kumwamba adziwa kuti musowa zonse zimenezo.

33 Koma muthange mwafuna Ufumu wace ndi cilungamo cace, ndipo zonse zimenezo zidzaonjezedwa kwa inu.

34 Cifukwa cace musadere nkhawa za mawa; pakuti mawa adzadzidera nkhawa iwo okha, Zikwanire tsiku zobvuta zace.

7

1 Musaweruze, kuti mungaweruzidwe.

2 Pakuti ndi kuweruza kumene muweruza nako, inunso mudzaweruzidwa; ndipo ndi muyeso umene muyesa nao, kudzayesedwa kwa inunso.

3 Ndipo upenya bwanji kacitsotso kali m'diso la mbale wako, koma mtanda uli m'diso la iwe mwini suuganizira?

4 Kapena udzati bwanji kwa mbale wako, Tandilola ndicotse kacitsotso m'diso lako; ndipo ona, mtandawo ulimo m'diso lakoli.

5 Wonyenga iwe! tayamba kucotsa m'diso lako mtandawo, ndipo pomwepo udzapenyetsa kucotsa kacitsotso m'diso la mbale wako.

6 Musamapatsa copatulikaco kwa agaru, ndipo musamaponya ngale zanu patsogolo pa nkhumba, kuti zingazipondereze ndi mapazi ao, ndi potembenuka zingang'ambe inu.

7 Pemphani, ndipo cidzapatsidwa kwa inu; funani, ndipo mudzapeza; gogodani, ndipo cidzatsegulidwa kwa inu;

8 pakuti yense wakupempha alandira; ndi wakufunayo apeza; ndi kwa wogogodayo citsegulldwa.

9 Kapena munthu ndani wa inu, amene pompempha mwana wace mkate, adzampatsa mwala?

10 Kapena pompempha nsomba, adzampatsa iye njoka kodi?

11 Comweco, ngati inu, muli oipa, mudziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, kopambana kotani nanga Atate wanu wa Kumwamba adzapatsa zinthu zabwino kwa iwo akumpempha Iye?

12 Cifukwa cace zinthu ziri zonse mukafuna kuti anthu acitire inu, inunso muwacitire iwo zotero; pakuti ico ndico cilamulo ndi aneneri.

13 Lowani pa cipata copapatiza; cifukwa cipata ciri cacikuru, ndi njira yakumuka nayo kukuonongeka iri yotakata; ndipo ali ambiri amene alowa pa ico.

14 Pakuti cipata ciri copapatiza, ndi icepetsa njirayo yakumuka nayo kumoyo, ndimo akucipeza cimeneco ali owerengeka.

15 Yang'anirani mupewe aneneri onyenga, amene adza kwa inu ndi zobvala zankhosa, koma m'kati mwao ali afisi alusa.

16 Mudzawazindikira ndi zipatso zao. Kodi achera mphesa paminga, kapena nkhuyu pamtula?

17 Comweco mtengo wabwino uli wonse upatsa zipatso zokoma; koma mtengo wamphuci upatsa zipatso zoipa,

18 Sungathe mtengo wabwino kupatsa zipatso zoipa, kapena mtengo wamphuci kupatsa zipatso zokoma.

19 Mtengo uli wonse wosapatsa cipatso cokoma, audula, nautaya kumoto.

20 Inde comweco pa zipatso zao mudzawazindikira iwo.

21 Si yense wakunena kwa Ine, Ambuye, Ambuye, adzalowa mu Ufumu wa Kumwamba; koma wakucitayo cifuniro ca Atate wanga wa Kumwamba.

22 Ambiri adzati kwa Ine tsiku lomwelo, Ambuye, Ambuye, kodi sitinanenera mau m'dzina lanu, ndi m'dzina lanunso kuturutsa mizimu yoipa, ndi kucita m'dzina lanunso zamphamvu zambiri?

23 Ndipo pamenepo ndidzafukulira iwo, Sindinakudziwani inu nthawi zonse; cokani kwa Ine, inu akucita kusayeruzika.

24 Cifukwa cimeneci yense amene akamva mau anga amenewa, ndi kuwacita, ndidzamfanizira iye ndi munthu wocenjera, amene anamanga nyumba yace pathanthwe;

25 ndipo inagwa mvula, nidzala mitsinje, ndipo zinaomba mphepo, zinagunda pa nyumbayo; koma siinagwa; cifukwa inakhazikika pathanthwepo.

26 Ndipo yense akamva mau anga amenewa, ndi kusawacita, adzafanizidwa ndi munthu wopusa, yemwe anamanga nyumba yace pamcenga;

27 ndipo inagwa mvula, nidzala mitsinje, ndipo zinaomba mphepo, zinagunda pa nyumbayo; ndipo inagwa; ndi kugwa kwace kunali kwakukuru.

28 Ndipo panakhala pamene Yesu anatha mau amenewa, makamu a anthu anazizwa ndi ciphunzitso cace:

29 pakuti anawaphunzitsa monga mwini mphamvu, wosanga alembiao.

8

1 Ndipo pakutsika pace paphiripo, inamtsata mipingo yambiri ya anthu.

2 Ndipo onani, wakhate anadza namgwadira Iye, nanena, Ambuye ngati mufuna mungathe kundikonza.

3 Ndipo Yesu anatambalitsa dzanja lace, namkhudza iye, nati, Ndifuna; takonzedwa. Ndipo pomwepo khate lace linacoka.

4 Ndipo Yesu ananena naye, Ona, iwe, usauze munthu; koma muka, udzionetse wekha kwa wansembe, nupereke mtulo umene anaulamulira Mose, ukhale mboni kwaiwo.

5 Ndipo m'mene Iye analowa m'Kapernao anadza kwa Iye kenturiyo, nampemba Iye,

6 nati, Ambuye, mnyamata wanga ali gone m'nyumba wodwala manjenje, wozunzidwa koopsa,

7 Ndipo Yesu ananena naye, Ndifika Ine, ndidzamciritsa iye.

8 Koma kenturiyoyo anabvomera nati, Ambuye, sindiyenera kuti mukalowe pansi pa chindwi langa iai; koma mungonena mau, ndipo adzaciritsidwa mnyamata wanga.

9 Pakuti inenso ndiri munthu wakumvera ulamuliro, ndiri nao asilikari akundimvera ine: ndipo ndinena kwa uyu, Muka, namuka; ndi kwa wina, Idza, nadza; ndi kwa kapolo wanga, Cita ici, nacita.

10 Ndipo pakumva ici, Yesu anazizwa, nati kwa iwo akumtsata, Indetu ndinena kwa inu, ngakhale mwa Israyeli, sindinapeza cikhulupiriro cotere.

11 Ndipo ndinena ndi inu, kuti ambiri a kum'mawa ndi a kumadzulo adzafika, nadzakhala pamodzi ndi Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo, mu Ufumu wa Kumwamba;

12 koma anawo a Ufumu adzatayidwa ku mdima wakunja; komweko kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.

13 Ndipo Yesu anati kwa kenturiyoyo, Pita, kukhale kwa iwe monga unakhulupirira. Ndipo anaciritsidwa mnyamatayo nthawi yomweyo.

14 Ndipo pofika Yesu ku nyumba ya Petro, anaona mpongozi wace ali gone, alikudwala malungo.

15 Ndipo anamkhudza dzanja lace, ndipo malungo anamleka mkaziyo; ndipo anauka, namtumikira Iye.

16 Ndipo pakudza madzulo, anabwera nao kwa Iye anthu ambiri ogwidwa ndi mizimu yoipa; ndipo Iye anaturutsa mizimuyo ndi mau, naciritsa akudwala onse;

17 kotero kuti cikwaniridwe conenedwa ndi Yesaya mneneri, kuti, Iye yekha anatenga zofoka zathu, Nanyamula nthenda zathu.

18 Ndipo Yesu, poona makamu ambiri a anthu akumzungulira Iye, analamulira ophunzira amuke ku tsidya lina,

19 Ndipo anadza munthu mlembi, nati kwa Iye, Mphunzitsi, ndidzakutsatani Inu kuli konse mumukako.

20 Ndipo Yesu ananena kwa iye, Ankhandwe ali nazo nkhwimba zao, ndi mbalame za m'mlengalenga zisa zao, koma Mwana wa munthu alibe potsamira mutu wace.

21 Ndipo wina wa ophunzira ace anati kwa Iye, Ambuye, mundilole ine nditange ndamuka kuika maliro a atate wanga.

22 Koma Yesu ananena kwa iye, Tsata Ine, nuleke akufa aike akufa ao.

23 Ndipo pamene Iye atalowa m'ngalawa, ophunzira ace anamtsata Iye.

24 Ndipo onani, m panauka namondwe wamkuru panyanja, kotero kuti ngalawa inapfundidwa ndi mafunde: koma Iye anali m'tulo.

25 Ndipo iwo anadza, namuutsa Iye, nanena, Ambuye, tipulumutseni, tirikutayika.

26 Ndipo ananena Iye kwa iwo, Muli amantha bwanji, okhulupirira pang'ono inu? Pomwepo Iye anauka, nadzudzula mphepo ndi nyanja, ndipo panagwa bata lalikuru.

27 Ndipo anazizwa anthuwo nanena, Ndiye munthu wotani uyu, pakuti ngakhale mphepo ndi nyanja zimvera Iye?

28 Ndipo pofika Iye ku tsidya lina, ku dziko la Agadara, anakomana naye awiri ogwidwa ndi ziwanda, akuturuka kumanda, aukali ndithu, kotero kuti sangathe kupitapa munthu pa njira imeneyo.

29 Ndipo onani, anapfuula nati, Tiri nanu ciani, inu Mwana wa Mulungu? mwadza kuno kodi kutizunza ife, nthawi yace siinafike?

30 Ndipo panali patari ndi iwo gulu la nkhumba zambiri zirinkudya.

31 Ndipo mizimuyo inampempha Iye ninena, Ngati mutiturutsa, mutitumize ife tilowe m'gulu la nkhumbazo.

32 Ndipo anati kwa iyo, Mukani. Ndipo inaturuka, nimuka, kukalowa m'nkhumbazo; ndipo onani, gulu lonse linathamangira kunsi kuphompho m'nyanjamo, ndipo linafa m'madzi.

33 Koma akuziweta anathawa, namuka kumidzi, nauza zonse, ndi zakuti zao za aziwanda aja.

34 Ndipo onani, mudzi wonse unaturukira kukakumana naye Yesu, ndipo m'mene anamuona Iye, anampempha kuti acoke m'malire ao.

9

1 Ndipo Iye analowa m'ngalawa, naoloka, nadza kumudzi kwao.

2 Ndipo onani, anabwera naye kwa Iye munthu wamanjenje, wakugona pachika: ndipo Yesu pakuona cikhulupiriro cao, anati kwa wodwalayo, Limba mtima, mwana, macimo ako akhululukidwa.

3 Ndipo onani, ena a alembi ananena mumtima mwao, Uyu acitira Mulungu mwano.

4 Ndipo Yesu, pozindikira maganizo ao, anati, Cifukwa canji mulinkuganizira zoipam'mitimayanu?

5 pakuti capafupi nciti, kunena, Macimo ako akhululukidwa; kapena kunena, Tanyamuka nuyende?

6 Koma kuti mudziwe kuti ali nazo mphamvu Mwana wa munthu pansi pano za kukhululukira macimo (pomwepo ananena kwa wodwalayo), Tanyamuka, nutenge chika lako, numuke kunyumba kwako.

7 Ndipo ananyamuka, napita ku nyumba kwace.

8 Ndipo m'mene anthu a makamu anaciona, anaopa, nalemekeza Mulungu, wakupatsa anthu mphamvu yotere.

9 Ndipo Yesu popita, kucokera kumeneko, anaona munthu, dzina lace Mateyu, alinkukhala polandirira msonkho, nanena kwa iye, Nditsate Ine. Ndipo iye anauka, namtsata.

10 Ndipo panali pamene Iye analinkukhala pacakudya m'nyumba, onani, amisonkho ndi ocimwa ambiri anadza nakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ace.

11 Ndipo Afarisi, pakuona ici, ananena kwa ophunzira ace, Cifukwa ninji Mphunzitsi wanu alinkudya pamodzi ndi amisonkho ndi ocimwa?

12 Ndipo m'mene Yesu anamva anati, Olimba safuna sing'anga ai, koma odwala.

13 Koma mukani muphunzire nciani ici: Ndifuna cifundo, si nsembe ai; pakuti sindinadza kudzaitana olungama, koma ocimwa.

14 Pomwepo anadza kwa Iye ophunzira ace a Yohane, nati, Cifukwa ninji ife ndi Afarisi tisala kudya kawiri kawiri, koma ophunzira anu sasala?

15 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Nanga anyamata a nyumba ya ukwati angathe kulira kodi nthawi imene mkwati akhala nao? koma adzafika masiku, pamene mkwati adzacotsedwa kwa iwo, ndipo pomwepo adzasala kudya.

16 Ndipo kulibe munthu aphathika cigamba ca nsaru yaiwisi pa copfunda cakale; pakuti cigamba cace cizomoka ku copfundaco, ndipo cicita ciboo cacikuru.

17 Kapena samathira vinyo watsopano m'matumba akale; akatero, matumba aphulika, ndi vinyo atayika, ndi matumba aonongeka: koma athira vinyo watsopano m'matumba atsopano, ndi zonse ziwiri zisungika.

18 M'mene Iye analikulankhula nao zinthu zimenezo, onani, anadza munthu mkuru, namgwadira Iye, nanena, Wamwalira tsopanolimwana wanga wamkazi, komatu mudze muike dzanja lanu pa iye, ndipo adzakhala ndi moyo.

19 Ndipo Yesu ananyamuka namtsata iye, ndi ophunzira ace omwe.

20 Ndipo onani, mkazi, anali ndi nthenda yacidwalire zaka khumi ndi ziwiri, anadza pambuyo pace, nakhudza mphonje ya copfundacace;

21 pakuti analikunena mwa iye yekha, Ngati ndingakhudze copfunda cace cokha ndidzacira.

22 Koma Yesu potembenuka ndi kuona iye anati, Limba mtima, mwana wamkaziwe, cikhulupiriro cako cakuciritsa. Ndipo mkaziyo anacira kuyambira nthawi yomweyo.

23 Ndipo Yesu polowa m'nyumba yace ya mkuruyo, ndi poona oyimba zitoliro ndi khamu la anthu obuma,

24 ananena, Turukani, pakuti kabuthuko sikanafa koma kali m'tulo. Ndipo anamseka Iye pwepwete.

25 Koma pamene khamulo linaturutsidwa, Iye analowamo, nagwira dzanja lace; ndipo kabuthuko kadauka.

26 Ndipo mbiri yace imene inabuka m'dziko lonse limenelo.

27 Ndipo popita Yesu kucokera kumeneko, anamtsata Iye anthu awiri akhungu, opfuula ndi kuti, Muticitire ife cifundo, mwana wa Davide.

28 Ndipo m'mene Iye analowa m'nyumbamo, akhunguwo anadza kwa Iye; ndipo Yesu anati kwa iwo, Mukhulupirira kodi kuti ndikhoza kucita ici? Anena kwa Iye, Inde, Ambuye.

29 Pomwepo anakhudza maso ao, nati, Cicitidwe kwa inu monga cikhulupiriro canu.

30 Ndipo maso ao anaphenyuka. Ndipo Yesu anawauzitsa Iwo, nanena, Yang'anirani, asadziwe munthu ali yense.

31 Koma iwo anaturukamo, nabukitsa mbiri yace m'dziko lonselo.

32 Ndipo pamene iwo analikuturuka, onani, anabwera naye kwa Iye munthu wosalankhula, wogwidwa ndi ciwanda.

33 Ndipo m'mene cinaturutsidwa ciwandaco, wosalankhulayo analankhula, ndipo makamu a anthu anazizwa, nanena, Kale lonse sicinaoneke comweco mwa Israyeli.

34 Koma Afarisi analinkunena, Aturutsa ziwanda ndi mphamvu zace za mfumu ya ziwanda.

35 Ndipo Yesu anayendayenda m'mizinda yonse ndi m'midzi, namaphunzitsa m'masunagoge mwao, nalalikira uthenga wabwino wa Ufumuwo, naciritsa nthenda iri yonse ndi zofoka zonse.

36 Koma Iye, poona makamuwo, anagwidwa m'mtima ndi cisoni cifukwa ca iwo, popeza anali okambululudwa ndi omwazikana, akunga nkhosa zopanda mbusa.

37 Pomwepo ananena kwa ophunzira ace, Zotuta zicurukadi koma anchito ali owerengeka.

38 Cifukwa cace pempherani Mwini zotuta kuti akokose anchito kukututakwace.

10

1 Ndipo pamene Iye anadziitanira ophunzira ace khumi ndi awiri, anapatsa iwo mphamvu pa mizimu yoipa, yakuiturutsa, ndi yakuciza nthenda iri yonse ndi zofoka zonse.

2 Ndipo maina ao a atumwiwo khumi ndi awiri ndi awa: woyamba Simoni wochedwa Petro, ndi Andreya mbale wace; Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi Yohane mbale wace;

3 Filipo, ndi Bartolomeyo; Tomasi, ndi Mateyu wamsonkhoyo; Yakobo mwana wa Alifeyo, ndi Tadeyo;

4 Simoni Mkanani, ndi Yudasi Isikariote amenenso anampereka Iye.

5 Awa amene, khumi ndi awiriwa, Yesu anawatumiza, nawalangiza ndi kuti, Musapite ku njira ya kwa anthu akunja, ndi m'mudzi wa Asamariya musamalowamo:

6 koma makamaka mupite ku nkhosa zosokera za banja la Israyeli.

7 Ndipo pamene mulikupita lalikani kuti, Ufumu wa Kumwamba wayandikira.

8 Ciritsani akudwala, ukitsani akufa, konzani akhate, turutsani ziwanda: munalandira kwaulere, patsani kwaulere.

9 Musadzitengere ndalama zagolidi, kapena zasiliva, kapena zakobiri m'malamba mwanu;

10 kapena thumba la kamba la kunjira, kapena malaya awiri, kapena nsapato, kapena ndodo; pakuti wanchito ayenera kulandira zakudya zace.

11 Ndipo m'mzinda uliwonse, kapena m'mudzi mukalowamo, mufunsitse amene ali woyenera momwemo; ndipo bakhalani komweko kufikira muturukamo.

12 Ndipo polowa m'nyumba muwalankhule.

13 Ndipo ngati nyumbayo iri yoyenera, mtendere wanu udze pa iyo, koma ngati siiri yoyenera, mtendere wanu ubwerere kwa inu.

14 Ndipo yemwe sadzakulandirani inu, kapena kusamva mau anu, pamene mulikuturuka m'nyumbayo, kapena m'mudzimo, sansani pfumbi m'mapazi anu.

15 Indetu ndinena kwa inu, kuti, tsiku la kuweruza, mlandu wao wa Sodomu ndi Gomora udzacepa ndi wace wa mudzi umenewo.

16 Taonani, Ine ndikutumizani inu monga nkhosa pakati pa afisi; cifukwa cace khalani ocenjera monga njoka, ndi oona mtima monga nkhunda.

17 Koma cenjerani ndi anthu; pakuti adzakuperekani inu kwa akuru a mlandu, nadzakukwapulani inu m'masunagoge mwao;

18 Ndiponso adzamuka nanu kwa akazembe ndi mafumu cifukwa ca Ine, kukhala mboni ya kwa iwo, ndi kwa anthu akunja.

19 Koma pamene pali ponse angakuperekeni inu, musamadera nkhawa mudzalankhule bwanji kapena mudzanene ciani; pakuti cimene mudzacilankhula, cidzapatsidwa kwa inu nthawi yomweyo;

20 pakuti wolankhula si ndinu, koma Mzimu wa Atate wanu akulankhula mwa inu.

21 Ndipo mbale adzapereka mbale wace kuimfa, ndi atate mwana wace: ndipo ana adzatsutsa akuwabala, nadzawafetsa iwo.

22 Ndipo adzada inu anthu onse cifukwa ca dzina langa; koma iye wakupirira kufikira cimariziro, iyeyu adzapulumutsidwa.

23 Koma pamene angakuzunzeni inu m'mudzi uwu, thawirani mwina: indetu ndinena kwa inu, Simudzaitha mizinda ya Israyeli, kufikira Mwana wa munthu atadza.

24 Wophunzira saposa mphunzitsi wace, kapena kapolo saposa mbuye wace.

25 Kumkwanira wophunzira kuti akhale monga mphunzitsi wace, ndi kapolo monga mbuye. Ngati anamucha mwini banja Beelzebule, sadzaposa kodi kuwatero apabanja ace?

26 Cifukwa cace musaopa iwo; pakuti palibe kanthu kanabvundikiridwa, kamene sikadzaululidwa; kapena kanthu kobisika, kamene sikadzadziwika.

27 Cimene ndikuuzani inu mumdima, tacinenani poyera; ndi cimene mucimva m'khutu, mucilalikire pa macindwi nyumba.

28 Ndipo musamaopa amene akupha thupi, koma moyo sangathe kuupha; koma makamaka muope Iye, wokhoza kuononga moyo ndi thupi lomwe m'gehena.

29 Kodi mpheta ziwiri sizigulidwa kakobiri? ndipo imodzi ya izo siigwa pansi popanda Atate wanu:

30 komatu inu, matsitsi onse a m'mutu mwanu awerengedwa.

31 Cifukwa cace musamaopa; inu mupambana mpheta zambiri.

32 Cifukwa cace yense amene adzabvomereza Ine pamaso pa anthu, Inenso nelidzambvomereza iye pamaso pa Atate wanga wa Kumwamba.

33 Koma 1 yense amene adzandikana Ine pamaso pa anthu, Inenso nelidzamkana iye pamaso pa Atate wanga wa Kumwamba.

34 2 Musalingalire kuti nelidadzera kuponya mtendere pa dziko lapansi; sinelinadzera kuponya mtendere, koma lupanga.

35 3 Pakuti ndinadza kusiyanitsa munthu ndi atate wace, ndi mwana wamkazi ndi amace, ndi mkazi wokwatiwa ndi mpongozi wace:

36 ndipo 4 apabanja ace a munthu adzakhala adani ace.

37 5 Iye wakukonda atate wace, kapena amace koposa Ine, sayenera Ine, ndipo iye wakukonda mwana wace wamwamuna, kapena wamkazi koposa Ine, sayenera Ine.

38 Ndipo 6 iye amene satenga mtanda wace, natsata pambuyo panga, sayenera Ine.

39 7 Iye amene apeza moyo wace, adzautaya; ndi iye amene ataya moyo wace, cifukwa ca Ine, adzaupeza.

40 8 Iye wakulandira inu, andilandira Ine, ndi wakundilandira Ine, amlandira Iye amene ananditumiza Ine.

41 9 Iye wakulandira mneneri, pa dzina la mneneri, adzalandira mphotho ya mneneri; ndipo wakulandira munthu wolungama, pa dzina la munthu wolungama, adzalandira mphotho ya munthu wolungama.

42 Ndipo 10 amenealiyense adzamwetsa mmodzi wa ang'ono awa cikho cokha ca madzi ozizira, pa dzina la wophunzira, indetu ndinena kwa inu, iye sadzataya mphotho yace.

11

1 Ndipo panali, pamene Yesu anatha kuwafotokozera ophunzira ace khumi Ndi awiri, Iye anacokera kumeneko kukaphunzitsa Ndi kulalikira m'midzi mwao.

2 Koma Yohane, pakumva m'nyumba yandende nchito za Kristu, anatumiza ophunzira ace mau,

3 nati kwa Iye, Inu ndinu wakudza kodi, kapena tiyembekezere wina?

4 Ndipo Yesu anayankha, nanena nao, Mukani mubwezere mau kwa Yohane zimene muzimva ndi kuziona:

5 akhungu alandira kuona kwao, Ndi opunduka miyendo ayenda, akhate akonzedwa, indi ogontha akumva, ndi akufa aukitsidwa, ndi kwa aumphawi ulalikidwa uthenga wabwino.

6 Ndipo wodala iye amene sakhumudwa cifukwa ca Ine.

7 Ndipo m'mene iwo analikumuka, Yesu anayambonena Ndi makamu a anthu za kwa Yohane, Munaturuka kunka kucipululu kukapenyanji? Bango logwedezeka nd: mphepo kodi?

8 Koma munaturuka kukaona ciani? Munthu wobvala zofewa kodi? Onani, akubvala zofewa alim'nyumba zamafumu.

9 Koma munaturukiranji? Kukaona mneneri kodi? Indetu, ndinena kwa inu, wakuposa mneneri.

10 Uyu ndiye amene kunalembedwa za iye, kuti, Onani Ine nditumiza mthenga wanga pa nkhope yanu, Amene adzakonza njira yanu m'tsogolo mwanu.

11 Indetu ndinena kwa inu, Sanauke wakubadwa mwa akazi munthu wamkuru woposa Yohane Mbatizi; koma iye amene ali wocepa mu Ufumu wa Kumwamba amkulira iye.

12 Ndipo kuyambira masiku a Yohane Mbatizi, kufikira tsopano lino, Ufumu wa Kumwamba uli wokangamizidwa, ndipo okangamirawo aukwatula ndi mphamvu.

13 Pakuti aneneri onse ndi cilamulo cinanenera kufikira pa Yohane.

14 Ndipo ngati mufuna kulandira, uyu ndiye Eliya amene amati akudza.

15 Amene ali ndi makutu akumva, amve.

16 Koma ndidzafanizira ndi ciani obadwa awa a makono? Ali ofanana ndi ana akukhala m'mabwalo a malonda, amene alikuitana anzao,

17 ndi kuti, Tinakulizirani inu zitoliro, ndipo inu simunabvina; tinabuma maliro, ndipo inu simunalira.

18 Pakuti Yohane anadza wosadya, wosamwa, ndipo iwo amati, Ali ndi ciwanda.

19 Mwana wa munthu anadza wakudya, ndi wakumwa, ndipo iwo amati, Onani munthu wakudyaidya ndi wakumwaimwa vinyo, bwenzi la amisonkho ndi ocimwa! Ndipo nzeru iyesedwa yolungama ndi nchito zace.

20 Pomwepo Iye anayamba kutonza midziyo, m'mene zinacitidwa zambiri za nchito zamphamvu zace, cifukwa kuti siinatembenuke.

21 Tsoka kwa iwe, Korazini! tsoka kwa iwe, Betsaida! cifukwa ngati zamphamvu zimene zacitidwa mwa inu zikadacitidwa m'Turo ndi m'Sidoni, akadatembenuka mtima kale kale m'ziguduli ndi m'phulusa.

22 Komanso ndinena kwa inu kuti dzuwa la kuweruza mlandu wao wa Turo ndi Sidoni udzacepa ndi wanu.

23 Ndipo iwe, Kapernao, udzakwezedwa kodi kufikira kuthambo? udzatsika kufikira ku dziko la akufa: cifukwa ngati zamphamvu zimene zacitidwa mwa iwe zikadacitidwa m'Sodomu, uyo ukadakhala kufikira lero.

24 Komanso ndinena kwa im kuti dzuwa la kuweruza, mlandu wace wa Sodomu udzacepa ndi wako.

25 Nyengo imeneyo Yesu anayankha nati, Ndibvomerezana ndi Inu, Atate, Mwini Kumwamba ndi dziko lapansi, kuti munazibisira izo kwa anzeru ndi akudziwitsa, ndipo munaziululira zomwe kwa makanda:

26 etu, Atate, cifukwa cotero cinakhala cokondweretsa pamaso panu.

27 Zinthu zonse zinaperekedwa kwa Ine ndi Atate wanga; ndipo palibe munthu adziwa Mwana, koma Atate yekha; ndi palibe wina adziwa Atate, koma M wana yekha, ndi iye amene Mwana afuna kumuululira.

28 Idzani kuno kwa Ine nonsenu akulema ndi akuthodwa, ndipo Ine ndidzakupumulitsani inu.

29 Senzani gori langa, ndipo phunzirani kwa Ine; cifukwa ndiri wofatsa ndi wodzicepetsa mtima: ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.

30 Pakuti 1 gori langa liri lofewa, ndi katundu wanga ali wopepuka.

12

1 Nyengo imeneyo Yesu anapita tsiku la Sabata pakati pa minda ya tirigu; ndipo ophunzira ace anali ndi njala, nayamba kubudula ngala, nadya.

2 Koma Afarisi, pakuona, anati kwa Iye, Tapenyani, ophunzira anu acita cosaloleka tsiku la Sabata.

3 Koma Iye anati kwa iwo, Kodi simunawerenga cimene anacicita Davide, pamene anali ndi njala, ndi iwo amene anali naye?

4 kuti analowa m'nyumba ya Mulungu, nadya mikate yoonetsa, imene yosaloleka kudya iye kapena amene anali naye, koma ansembe okha okha.

5 Kapena simunawerenga kodi m'cilamulo, kuti tsiku la Sabata ansembe m'Kacisi amaipitsa tsiku la Sabata, nakhala opanda cimo?

6 Koma ndinena kwa inu, kuti wakuposa Kacisiyo ali pompano.

7 Koma mukadadziwa nciani ici: Ndifuna cifundo, si nsembe ai; simukadaweruza olakwa iwo osacimwa,

8 pakuti Mwana wa munthu ali mwini tsiku la Sabata.

9 Ndipo Iye anacokera pamenepo, nalowa m'sunagoge mwao;

10 ndipo onani, munali munthu wa dzanja lopuwala, Ndipo anamfunsitsa Iye, ndi kuti, Nkuloleka kodi kuciritsa tsiku la Sabata? kuti ampalamulitse mlandu.

11 Koma Iye anati kwa iwo, Munthu ndani wa inu, amene ali nayo nkhosa imodzi, ndipo ngati idzagwa m'dzenje tsiku la Sabata, kodi sadzaigwira, ndi kuiturutsa?

12 Nanga kuposa kwace kwa munthu ndi nkhosa nkotani! Cifukwa ca ici nkuloleka kucita zabwino tsiku la Sabata.

13 Pomwepo ananena Iye kwa munthuyo, Tansa dzanja Lako. Ndipo iye analitansa, ndipo linabwezedwa lamoyo longa linzace.

14 Ndipo Afarisi anaturuka, nakhala upo womcitira Iye mwa kumuononga.

15 Koma Yesu m'mene anadziwa, anacokera kumeneko: ndipo anamtsata Iye anthu ambiri; ndipo Iye anawaciritsa iwo onse,

16 nawalimbitsira mau kuti asamuulule Iye;

17 kuti cikacitidwe conenedwa ndi Yesaya mneneri uja, kuti,

18 Taona mnyamata wanga, amene ndinamsankha, Wokondedwa wanga, amene moyo wanga ukondwera naye; Pa Iye ndidzaika Mzimu wanga, Ndipo Iye adzalalikira ciweruzo kwa akunja.

19 Sadzalimbana, sadzapfuula; Ngakhale mmodzi sadzamva mau ace m'makwalala;

20 Bango lophwanyika sadzalityola, Ndi nyali yofuka sadzaizima, Kufikira Iye adzatumiza ciweruzo cikagonjetse,

21 Ndipo akunja adzakhulupirira dzina lace.

22 Pomwepo anabwera naye kwa Iye munthu wogwidwa ndi ciwanda, wakhungu ndi wosalankhula; ndipo Iye anamciritsa, kotero kuti wosalankhulayo analankhula, napenya.

23 Ndipo makamu onse a anthu anazizwa, nanena, Uyu si mwana wa Davide kodi?

24 Koma Afarisi pakumva, anati, Uyu samaturutsa ziwanda koma ndi mphamvu yace ya Beelzebule, mkuru wa ziwanda.

25 Ndipo Yesu anadziwa maganizo ao, nati kwa iwo, Ufumu uti wonse wogawanika pa wokha sukhalira kupasuka, ndi mudzi uti wonse kapena banja logawanika pa lokha silidzakhala;

26 ndipo ngati Satana amaturutsa Satana, iye agawanika pa yekha; ndipo udzakhala bwanji ufumu wace?

27 Ndipo ngati Ine ndimaturutsa ziwanda ndi mphamvu yace ya Beelzebule, ana anu amaziturutsa ndi mphamvu ya yani? cifukwa cace iwo adzakhala oweruza anu.

28 Koma ngati Ine ndimaturutsa ziwanda ndi mphamvu yace ya Mzimu wa Mulungu, pomwepo Ufumu wa Mulungu unafika pa inu.

29 Kapena akhoza bwanji munthu kulowa m'banja la munthu wolimba, ndi kufunkha akatundu ace, ngati iye sayamba kumanga munthu wolimbayo? ndipo pamenepo adzafunkha za m'banja lace.

30 Iye wosakhala pamodzi ndi Ine akana Ine, ndi iye wosasonkhanitsa pamodzi ndi Ine amwazamwaza.

31 Cifukwa cace ndinena kwa inu, Macimo onse, ndi zonena zonse zamwano, zidzakhululukidwa kwa anthu; koma camwano ca pa Mzimu Woyera sicidzakhululukidwa.

32 Ndipo amene ali yense anganenere Mwana wa munthu zoipa, adzakhululukidwa; koma amene ali yense anganenere Mzimu Woyera zoipa sadzakhululukidwa nthawi yino kapena irinkudzayo.

33 Ukakoma mtengo, cipatso cace comwe cikoma; ukaipa mtengo, cipatso cace comwe ciipa; pakuti ndi cipatso cace mtengo udziwika.

34 Akubadwa inu a njoka, mungathe bwanji kulankhula zabwino, inu akukhala oipa? pakuti m'kamwa mungolankhula mwa kusefuka kwace kwa mtima.

35 Munthu wabwino aturutsa zabwino m'cuma cace cabwino, ndi munthu woipa aturutsa zoipa m'cuma cace coipa.

36 Ndipo ndinena kwa inu, kuti mau onse opanda pace, amene anthu adzalankhula, adzawawerengera mlandu wace tsiku la kuweruza.

37 Pakuti udzayesedwa wolungama ndi mau ako, ndipo ndi mau ako omwe udzatsutsidwa.

38 Pomwepo alembi ndi Afarisi ena anayankha Iye nati, Mphunzitsi, tifuna kuona cizindikiro ca Inu.

39 Koma Iye anayankha nati kwa iwo, Akubadwa oipa acigololo afunafuna cizindikiro; ndipo sicidzapatsidwa kwa iwo cizindikiro, komatu cizindikiro ca Yona mneneri;

40 pakuti monga Yona anali m'mimba mwa cinsomba masiku atatu ndi usiku wace, comweco Mwana wa munthu adzakhala mumtima mwa dziko lapansi masiku atatu ndi usiku wace.

41 1 Anthu a ku Nineve adzauka pamlandu pamodzi ndi obadwa amakono, nadzawatsutsa; cifukwa 2 iwo anatembenuka mtima ndi kulalikira kwace kwa Yona; ndipo onani, wakuposa Y ona ali pano.

42 3 Mfumu yaikazi ya kumwera adzauka pamlandu pamodzi ndi obadwa amakono, nadzawatsutsa; cifukwa iye anacokera ku mathero a dziko lapansi kudzamva nzeru ya Solomo; ndipo onani, wakuposa Solomo ali pano.

43 Koma mzimu wonyansa, utaturuka mwa munthu, umapitirira malo opanda madzi kufunafuna mpumulo, osaupeza.

44 Pomwepo unena, ndidzabwerera kunka kunyumba kwanga, konkuja ndinaturukako; ndipo pakufikako uipeza yopanda wokhalamo, yosesedwa ndi yokonzedwa.

45 Pomwepo upita, nutenga pamodzi ndi uwu mizimu yina inzace isanu ndi iwiri yoipa yoposa mwini yekhayo, ndipo ilowa, nikhalamo. Ndipo 4 matsirizidwe ace a munthu uyo akhala oipa oposa mayambidwe ace. Kotero kudzakhalanso kwa obadwa oipa amakono.

46 Pamene Iye anali cilankhulire ndi makamu, onani, amace ndi 5 abale ace anaima panja, nafuna kulankhula naye.

47 Ndipo munthu anati kwa Iye, Onani, amai wanu ndi abale anu aima pabwalo, nafuna kulankhula nanu.

48 Koma Iye anayankha, nati kwa iye wonenayo, Amai wanga ndani? ndi abale anga ndi ayani?

49 Ndipo anatambalitsa dzanja lace pa ophunzira ace, nati, Penyani amai wanga ndi abale anga!

50 Pakuti 6 ali yense amene adzacita cifuniro ca Atate wanga wa Kumwamba, yemweyo ndiye mbale wanga, ndi mlongo wanga, ndi amai wanga.

13

1 Tsiku lomwelo Yesu anaturuka m'nyumbamo, nakhala pansi m'mbali mwa nyanja.

2 Ndipo makamu ambiri a anthu anasonkhanira kwa Iye, kotero kuti Iye analowa m'ngalawa, nakhala pansi, ndipo khamu lonse linaima pamtunda.

3 Ndipo Iye anawauzira zinthu zambiri m'mafanizo, nanena, Onani, wofesa anaturuka kukafesa mbeu,

4 Ndipo m'kufesa kwace zina zinagwa m'mbali mwa njira, ndipo zinadza mbalame, nizilusira izo.

5 Koma zina zinagwa pamiyala, pamene panalibe dothi lambiri; ndipo pomwepo zinamera, pakuti sizinakhala nalo dothi lakuya, Ndipo m'mene dzuwa linakwera zinapserera;

6 ndipo popeza zinalibe mizu zinafota.

7 Koma zina zinagwa paminga, ndipo mingayo inayanga, nizitsamwitsa izo.

8 Koma zina zinagwa pa nthaka yabwino, ndipo zinabala zipatso, zina za makumi khumi, zina za makumi asanu ndi limodzi, zina za makumi atatu.

9 Amene ali ndi makutu, amve.

10 Ndipo ophunzirawo anadza, nati kwa Iye, Cifukwa canji muphiphiritsira iwo m'mafanizo?

11 Ndipo Iye anayankha nati, Cifukwa kwapatsidwa kwa inu kudziwa zinsinsi za Ufumu wa Kumwamba, koma sikunapatsidwa kwa iwo.

12 Pakuti yense amene ali nazo, kudzapatsidwa kwa iye, ndimo adzakhala nazo zocuruka; koma yense amene alibe, cingakhale comwe ali naco cidzacotsedwa kwa iye.

13 Cifukwa cace ndiphiphiritsira iwo m'mafanizo; cifukwa kuti akuona samaona, ndi akumva samamva, kapena samadziwitsa.

14 Ndipo adzacitidwa kwa iwo mau adanenera Yesaya, amene ati. Pakumva mudzamva, ndipo simudzazindikira konse; Pakupenya mudzapenya, ndipo simudzaona konse;

15 Cifukwa unalemera mtima wa anthuawa, Ndipo m'makutu ao anamva mogontha, Ndipo maso ao anatsinzina; Kuti asaone konse ndi maso, Asamve ndi makutu, Asazindikire ndi mtima wao, Asatembenuke, Ndipo ndisawaciritse iwo.

16 Koma maso anu ali odala, cifukwa apenya; ndi makutu anu cifukwa amva.

17 Pakuti indetu ndinena kwa inu, kuti aneneri ambiri ndi anthu olungama analakalaka kupenya zimene muziona, koma sanaziona; ndi kumva zimene muzimva, koma sanazimva.

18 Ndipo tsono mverani inu fanizolo la wofesa mbeu uja.

19 Munthu ali yense wakumva mau a Ufumu, osawadziwitsai, woipayo angodza, nakwatula cofesedwaco mumtima mwace. Uyo ndiye wofesedwa m'mbali mwa njira.

20 Koma iye amene afesedwa pamiyala, uyu ndiye wakumva mau, ndi kuwalandira pomwepo ndi kusekera;

21 ndipo alibe mizu mwa iye, koma akhala nthawi yaing'ono; ndipo pakudza nsautso kapena zunzo cifukwa ca mau, iye akhumudwa pomwepo.

22 Ndipo iye amene afesedwa kuminga, uyu ndiye wakumva mau; ndipo kulabadira kwa dziko lapansi, ndi cinyengo ca cuma citsamwitsa mau, ndipo akhala wopanda cipatso.

23 Ndipo iye amene afesedwa pa nthaka yabwino, uyu ndiye wakumva mau nawadziwitsa; amene abaladi zipatso, nazifitsa, ena za makumi khumi, ena za makumi asanu ndi limodzi, ena za makumi atatu.

24 Fanizo lina Iye anawafotokozera iwo, nanena, Ufumu wa Kumwamba ufanizidwa ndi munthu, amene anafesa mbeu zabwino m'munda mwace;

25 koma m'mene anthu analinkugona, mdani wace anadza, nafesa namsongole pakati pa tirigu, nacokapo.

26 Koma pamene mmera unakula, nubala cipatso, pomwepo anaonekeranso namsongole.

27 Ndipo anyamata ace a mwini nyumbayo anadza, nati kwa iye, Mbuye, kodi simunafesa mbeu zabwino m'munda mwanu? nanga wacokera kuti namsongoleyo?

28 Ndipo iye ananena kwa iwo, Munthu mdani wanga wacicita ici. Ndipo anyamata anati kwa iye, Kodi mufuna tsopano kuti timuke, tikamsonkhanitse uyo pamodzi?

29 Koma iye anati, lai, kuti kapena m'mene mukasonkhanitsa namsongoleyo, mungazulenso tirigu pamodzi naye.

30 Kazilekeni zonse ziwiri, zikulire pamodzi kufikira pakututa; ndimo m'nyengo yakututa ndidzauza akututawo, Muyambe kusonkhanitsa namsongole, mummange uyu mitolo kukamtentha, koma musonkhanitse tirigu m'nkhokwe yanga.

31 Fanizo lina Iye anawafotokozera iwo, nanena, Ufumu wa Kumwamba uli wofanafana ndi kambeu kampiru, kamene anakatenga munthu, nakafesa pamunda pace;

32 kamene kakhaladi kakang'ono koposa mbeu zonse, koma katakula, kali kakakuru kuposa zitsambazonse, nukhala mtengo, kotero kuti mbalame za mlengalenga zimadza, nizibindikira mu nthambi zace.

33 Fanizo lina ananena kwa iwo; Ufumu wa Kumwamba uli wofanafana ndi cotupitsa mikate, cimene mkazi anacitenga, nacibisa m'miyeso itatu ya ufa, kufikira wonse unatupa.

34 Zonsezi Yesu anaziphiphiritsira m'mafanizo kwa makamu anthu; ndipo kopanda fanizo sanalankhula kanthu kwa iwo;

35 kuti cikacitidwe conenedwa ndi mneneri, kuti, Ndidzatsegula pakamwa panga ndi mafanizo; Ndidzaulula zinthu zobisika ciyambire kukhazikidwa kwace kwa dziko lapansi.

36 Pomwepo Iye anasiya makamuwo, nalowa m'nyumba; ndimo ophunzira ace anadza kwa Iye, nanena, Mutitanthauzire fanizo lija la namsongole wa m'munda.

37 Ndipo Iye anayankha nati, Wofesa mbeu yabwino ndiye Mwana wa munthu;

38 ndipo munda ndiwo dziko lapansi; ndi mbeu yabwino ndiyo ana a Ufumuwo; ndi namsongole ndiye ana a woipayo;

39 ndipo mdani amene anamfesa uwu ndiye mdierekezi: ndi kututa ndico cimariziro ca nthawi ya pansi pano; ndi otutawo ndiwo angelo.

40 Ndipo monga namsongole asonkhanitsidwa pamodzi, natenthedwa pamoto, matero mudzakhala m'cimariziro ca nthawi ya pansi pano.

41 Mwana wa munthu adzatuma angelo ace, ndipo iwo adzasonkhanitsa pamodzi, ndi kucotsa mu Ufumu wace zokhumudwitsa zonse, ndi anthu akucita kusayeruzika,

42 ndipo adzawataya iwo m'ng'anjo yamoto; kumeneko kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.

43 Pomwepo olungamawo adzawalitsa monga dzuwa, mu Ufumu wa Atate wao. Amene ali ndi makutu amve.

44 Ufumu wa Kumwamba uli wofanana ndi cuma cobisika m'munda; cimene munthu anacipeza, nacibisa; ndipo m'kucikonda kwace acoka, nagulitsa zonse ali nazo, nagula munda umenewu.

45 Ndiponso Ufumu wa Kumwamba uli wofanana ndi munthu wa malonda, wakufuna ngale zabwino:

46 ndipo m'mene anaipeza ngale imodzi ya mtengo wapatari, anapita, nagulitsa zonse anali nazo, naigula imeneyo.

47 Ndiponso, Ufumu wa Kumwamba uli wofanana ndi khoka loponyedwa m'nyanja, ndi 1 kusonkhanitsa pamodzi za mitundu yonse;

48 limene podzala, analibvuulira pamtunda; ndipo m'mene anakhala pansi, anazisonkhanitsa zabwino m'zotengera, koma zoipa anazitaya kuthengo.

49 Padzatero pa cimariziro ca nthawi ya pansi pano: angelo adzaturuka, 2 nadzawasankhula oipa pakati pa abwino,

50 nadzawataya m'ng'anjo yamoto; komweko kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.

51 Mwamvetsa zonsezi kodi? lwo anati kwa Iye, inde.

52 Ndipo Iye anati kwa iwo, Cifukwa cace, mlembi ali yense, wophunzitsidwa mu Ufumu wa Kumwamba, ali wofanana ndi munthu mwini banja, amene aturutsa m'cuma cace zinthu zakale ndi zatsopano.

53 Ndipo panali, pamene Yesu anatha mafanizo awa, anacokera kumeneko.

54 Ndipo 3 pofika ku dziko la kwao, anaphunzitsa iwo m'sunagoge mwao, kotero kuti anazizwa, nanena, Uyu adazitengakuti nzeru zimenezi ndi zamphamvu izi?

55 4 Kodi uyu si mwana wa mmisiri wa mitengo? kodi dzina lace la amace si Mariya? ndi 5 abale ace si Yakobo ndi Yosefe ndi Simoni ndi Yuda?

56 Ndipo alongo ace sali ndife onsewa? Ndipo iyeyo adazitenga zinthu zonsezi kuti?

57 Ndipo iwo anakhumudwa cifukwa ca Iye. Koma Yesu anati kwa iwo, 6 Mneneri sakhala wopanda ulemu koma ku dziko la kwao ndiko, ndi kubanja kwace.

58 Ndipo Iye, cifukwa ca kusakhulupirira kwao, sanacita kumeneko zamphamvu zambiri.

14

1 Nthawi imeneyo Herode mfumu anamva mbiri ya Yesu,

2 nanena kwa anyamata ace, U yo ndiye Yohane Mbatizi; anauka kwa akufa; ndipo cifukwa ca ici zamphamvuzi zilimbalimba mwa iye.

3 Pakuti Herode adamgwira Yohane, nammanga, namuika m'nyumba yandende cifukwa ca Herodiya, mkazi wa mbale wace Filipo.

4 Pakuti Yohane ananena kwa iye, Sikuloledwa kwa iwe kukhala naye.

5 Ndipo pofuna kumupha iye, anaopa khamu la anthu, popeza anamuyesa iye mneneri.

6 Koma pakufika tsiku la kubadwa kwace kwa Herode, mwana wamkazi wa Herodiya anabvina pakati pao, namkondweretsa Herode.

7 Pomwepo iye anamlonjeza cilumbirire, kumpatsa iye cimene ciri conse akapempha.

8 Ndipo iye, atampangira amace, anati, Ndipatseni ine kuno m'mbizi mutu wa Yohane Mbatizi. Ndipo mfumuyo anagwidwa ndi cisoni;

9 koma cifukwa ca malumbiro ace, ndi ca iwo anali naye pacakudya, analamulira upatsidwe;

10 ndipo anatumiza mnyamata, namdula mutu Yohane m'nyumba yandende.

11 Ndipo anautenga mutu wace m'mbizimo, naupatsa buthulo: ndipo iye anamuka nao kwa amace.

12 Ndipo ophunzira ace anadza, natola mtembo, nauika; ndipo anadza nauza Yesu.

13 Ndipo Yesu pakumva, anacokera kumeneko m'ngalawa, kunka ku malo acipululu pa yekha; ndipo makamu, pamene anamva, anamtsata Iye mumtunda kucokera m'midzi.

14 Ndipo Iye anaturuka, naona khamu lalikuru la anthu, nacitira iwo cifundo, naciritsa akudwala ao.

15 Ndipo pamene panali madzulo, ophunzira ace anafika kwa Iye, nanena, Malo ano nga cipululu, ndipo nthawi yapita tsopano; kauzeni makamuwo amuke, apite ku midzi kukadzigulira okha kamba.

16 Koma Yesu anati kwa iwo, Iwo alibe cifukwa ca kumukira, apatseni ndinu adye.

17 Koma iwo ananena kwa Iye, Ife tiribe kanthu pano koma mikate isanu, ndi nsomba ziwiri.

18 Ndipo Iye anati, Mudze nazo kuno kwa Ine.

19 Ndipo Iye analamulira makamu a anthu akhale pansi pamaudzu; ndipo Iye anatenga mikate isanuyo ndi nsomba ziwirizo, ndipo m'mene anayang'ana kumwamba, anadalitsa, nanyema, napatsa mikateyo kwa ophunzira, ndi ophunzira kwa makamuwo.

20 Ndipo anadya onse, nakhuta; ndipo anatola makombo otsala, mitanga khumi ndi iwiri yodzala.

21 Ndipo anadyawo anali amuna monga zikwi zisanu, kuwaleka akazi ndi ana.

22 Ndipo pomwepo Iye anafulumiza ophunzira alowe m'ngalawa, ndi kumtsogolera Iye ku tsidya lija, kufikira Iye atauza makamu amuke.

23 Ndipo pamene Iye anawauza makamuwo, anakwera m'phiri pa yekha, kukapemphera: ndipo pamene panali madzulo, Iye anakhala kumeneko yekha.

24 Koma pomwepo ngalawa idafika pakati pa nyanja, yozunzika ndi mafunde; pakuti mphepo inadza mokomana nao.

25 Ndipo pa ulonda wacinai wa usiku, Iye anadza kwa iwo, nayenda pamwamba pa nyanja.

26 Koma m'mene ophunzirawo anamuona Iye, alikuyenda pamadzi, ananthunthumira, nati, ndi mzukwa! Ndipo anapfuula ndi mantha.

27 Koma pomwepo Yesu analankhula nao, nati, Limbani mtima; ndine; musaope.

28 Ndipo Petro anamyankha Iye nati, Ambuye, ngati ndinutu, mundiuze ndidze kwa lou pamadzi.

29 Ndipo Iye anati, Idza, Ndipo Petro anatsika m'ngalawa, nayenda pamadzi, kufika kwa Yesu.

30 Koma m'mene iye anaiona mphepo, ana, opa; ndipo poyamba kunura, anapfuula, nati, Ambuye, ndipulumutseni ine!

31 Ndipo pomwepo Yesu anatansa dzanja lace, namgwira iye, nanena naye, Iwe wokhulupirira pang'ono, wakayikiranji mtima?

32 Ndipo pamene iwo analowa m'ngalawamo, mphepo inaleka.

33 Ndipo iwo amene anali m'ngalawamo anamgwadira, nanena, Zoonadi, ndinu Mwana wa Mulungu.

34 Ndipo pamene iwo anaoloka, anafika kumtunda, ku Genesarete.

35 Ndipo m'meneamuna a pamenepo anamzindikira, anatumiza konse ku dziko lonse lozungulira, nadzanao kwa Iye onse akukhala ndi nthenda;

36 ndipo anampempha Iye, kuti akhudze yokha mphonje ya cobvala cace; ndipo onse amene anamkhudza anaciritsidwa.

15

1 Pomwepo anadza kwa Yesu Afarisi ndi alembi, ocokera ku Yerusalemu, nati,

2 Ophunzira anu alumphiranji miyambo ya makolo? pakuti sasamba manja pakudya.

3 Ndipo Iye anayankha, nati kwa iwo, Inunso mulumphiranji lamulo la Mulungu cifukwa ca miyambo yanu?

4 Pakuti Mulungu anati, Lemekeza atate wako ndi amako; ndipo, Wakunenera atate wace ndi amace zoipa, afe ndithu.

5 Koma inu munena, Amene ali yense anena kwa atate wace kapena kwa amace, Ico ukanathandizidwa naco, neoperekedwa kwa Mulungu;

6 iyeyo sadzalemekeza atate wace. Ndipo inu mupeputsa mau a Mulungu cifukwa ca miyambo yanu.

7 Onyenga inu! Yesaya ananenera bwino za inu, ndikuti,

8 Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao; Koma mtima wao uli kutari ndi Ine.

9 Koma andilambira Ine kwacabe, Ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.

10 Ndipo Iye anaitana makamuwo nati kwa iwo, Imvani, nimudziwitse;

11 si cimene cilowa m'kamwa mwace ciipitsa munthu; koma cimene cituruka m'kamwa mwace, ndico ciipitsa munthu.

12 Pomwepo anadza ophunzira, nanena kwa Iye, Mudziwa kodi kuti Afarisi anakhumudwa pakumva conenaco?

13 Koma Iye anayankha nati, Mmera wonse, umene Atate wanga wa Kumwamba sanaubzala, udzazulidwa.

14 Kawalekeni iwo, ali atsogoleri akhungu. Ndipo ngati wakhungu amtsogolera wakhungu, onse awiri adzagwa m'mbuna.

15 Ndipo Petro anayankha nati kwa Iye, Mutifotokozere ife fanizoli.

16 Ndipo Iye anati, Kodi inunso mukhala cipulukirire?

17 Simudziwa kodi kuti zonse zakulowa m'kamwa zipita m'mimba, ndipo zitayidwa kuthengo?

18 Koma zakuturuka m'kamwa zicokera mumtima; ndizo ziipitsa munthu.

19 Pakuti mumtima mucokera maganizo oipa, zakupha, zacigololo, zaciwerewere, zakuba, za umboni wonama, zamwano;

20 izi ndizo ziipitsa munthu, koma kudya osasamba manja sikuipitsa munthuai.

21 Ndipo Yesu anaturukapo napatukira ku mbali za Turo ndi Sidoni.

22 Ndipo onani, mkazi wa ku Kanani anaturuka m'malire, napfuula, nati, Mundicitire ine cifundo Ambuye, mwana wa Davide; mwana wanga wamkazi wagwidwa koopsa ndi ciwanda.

23 Koma Iye sanamyankha mau amodzi. Ndipo ophunzira ace anadza, nampempha, nati, Mumuuze amuke; pakuti apfuula pambuyo pathu.

24 Ndipo Iye anayankha, nati, Sindinatumidwa kwa ena koma kwa nkhosa zotayika za banja la Israyeli.

25 Koma iye anadza, namgwadira Iye, nanena, Ambuye, ndithangateni ine.

26 Ndipo Iye anayankha, nati, Sicabwino kutenga mkate wa ana, ndi kuuponyera tiagaru.

27 Koma iye anati, Etu, Ambuye, pakutinso tiagaru timadya nyenyeswa zakugwa pagome pa ambuye ao.

28 Pomwepo Yesu anayankha, nati kwa iye, Mkaziwe, cikhulupiriro cako ndi cacikuru; cikhale kwa iwe monga momwe wafunira. Ndipo mwana wace anacira nthawi yomweyo.

29 Ndipo Yesu anacoka kumeneko, nadza ku nyanja ya Galileya, nakwera m'phiri, nakhala pansi pamenepo.

30 Ndipo makamu ambiri a anthu anadza kwa Iye, ali nao opunduka miyendo, akhungu, osalankhula, opunduka ziwalo, ndi ena ambiri, nawakhazika pansi pa mapazi ace: ndipo Iye anawaciritsa;

31 kotero kuti khamulo linazizwa, pakupenya osalankhula nalankhula, opunduka ziwalo nacira, ndi opunduka miyendo nayenda, ndi akhungu napenya, ndipo iwo analemekeza Mulungu wa Israyeli.

32 Ndipo Yesu anaitana ophunzira ace, nati, Mtima wanga ucitira cifundo khamu la anthuwa, pakuti ali cikhalire ndi Ine masiku atatu, ndipo alibe kanthu kakudya, ndipo sindifuna kuwauza iwo amuke osadya, kuti angaziye panjira,

33 Ndipo ophunzira ananena kwa Iye, Tiione kuti mikate yotere m'cipululu yakukhutitsa unyinji wotere wa anthu?

34 Ndipo Yesu ananena kwa iwo, Muli nayo mikate ingati? Ndipo iwo anati, Isanu ndi iwiri, ndi tinsomba pang'ono.

35 Ndipo Iye analamulira anthuwo akhale pansi onse;

36 natenga mikateyo isanu ndi iwiri ndi nsombazo; nayamika Mulungu, nanyema, napatsa kwa ophunzira, ndi ophunzira kwa anthu.

37 Ndipo onsewa anadya, nakhuta: ndipo anatola makombo otsala malicero asanu ndi awiri odzala.

38 Ndipo anadyawo anali amuna zikwi zinai kuwaleka akazi ndi ana.

39 Ndipo m'mene Iye anauza makamuwo amuke, analowa m'ngalawa, nafika m'malire Magadani.

16

1 Ndipo Afarisi ndi Asaduki anadza, namuyesa, namfunsa Iye awaonetse cizindikiro ca Kumwamba.

2 Koma Iye anayankha, nati kwa iwo, Madzulo munena, Kudzakhala ngwe; popeza thambo liri laceza.

3 Ndipo m'mawa, Lero nkwa mphepo; popeza thambo liri la ceza codera. Mudziwa kuzindikira za pa nkhope ya thambo; koma zizindikiro za nyengo yin o, simungathe kuzindikira.

4 Obadwa oipa ndi acigololo afunafuna cizindikiro; ndipo sadzalandira cizindikiro cina, koma cizindikiro ca Yona. Ndipo Iye anawasiya, nacokapo.

5 Ndipo ophunzira anadza ku tsidya linalo, naiwala kutenga mikate.

6 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Yang'anirani mupewe cotupitsa mkate ca Afarisi ndi Asaduki.

7 Ndipo iwo anafunsana wina ndi mnzace, nati, Sitinatenga mikate.

8 Koma Yesu, m'mene anadziwa, anati, Ha, inu okhulupirira pang'ono, mufunsana cifukwa ninji wina ndi mnzace, kuti simunatenga mikate?

9 kodi cikhalire simudziwa, ndipo simukumbukira mikate isanu ija ya anthu aja zikwi zisanu, ndi mitanga ingati munaitola?

10 Penanso mikate isanu ndi iwiri ija ya anthu zikwi zinai, ndi malicero angati munawatola?

11 Bwanji nanga simudziwa kuti sindinanena kwa inu za mikate? Koma pewani cotupitsa ca Afarisi ndi Asaduki.

12 Pomwepo anadziwitsa kuti sanawauza kupewa cotupitsa ca mikate, koma ciphunzitso ca Afarisi ndi Asaduki.

13 Ndipo Yesu, pamene anadza ku dziko la ku Kaisareya wa Filipi, anafunsa ophunzira ace, kuti, Anthu anena kuti Mwana wa munthu ndiye yani?

14 Ndipo iwo anati, Ena ati, Yohane Mbatizi; koma ena, Eliya; ndipo enanso Yeremiya, kapena mmodzi wa aneneri.

15 Iye ananena kwa iwo, Koma inu mutani kuti Ine ndine yani?

16 Ndipo Simoni Petro anayankha nati, Inu ndinu Kristu, Mwana wa Mulungu wamoyo.

17 Ndipo Yesu anayankha iye, nati, Ndiwe wodala, Simoni Bar-Yona: pakuti thupi ndi mwazi sizinakuululira ici, koma Atate wanga wa Kumwamba.

18 Ndiponso Ine ndinena kwa iwe, kuti iwe ndiwe Petro, ndipo pa thanthwe ili ndidzakhazika Mpingo wanga; ndipo makomo a dziko la akufa sadzaulaka uwo.

19 Ndidzakupatsa mafungulo a Ufumu wa Kumwamba; ndipo cimene ukamanga pa dziko lapansi cidzakhala comangidwa Kumwamba: ndipo cimene ukacimasula pa dziko lapansi, cidzakhala comasulidwa Kumwamba.

20 Pamenepo analamulira ophunzira kuti asauze munthu kuti Iye ndiye Kristu.

21 Kuyambira pamenepo Yesu anayamba kuwalangiza ophunzira ace, kuti kuyenera Iye amuke ku Yerusalemu, kukazunzidwa zambiri ndi akuru, ndi ansembe akuru, ndi alembi; ndi kukaphedwa, ndi tsiku lacitatu kuuka kwa akufa.

22 Ndipo Petro anamtenga Iye, nayamba kumdzudzula, kuti, Dzicitireni cifundo, Ambuye; sicidzatero kwa Inu ai.

23 Koma Iye anapotoloka, nati kwa Petro, Pita kumbuyo kwanga, Satana iwe; ndiwe condikhumudwitsa Ine; cifukwa sumasamalira za Mulungu, koma za anthu.

24 Pomwepo Yesu anati kwa ophunzira ace, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikane yekha, natenge mtanda wace, nanditsate Ine.

25 Pakuti iye amene afuna kupulumutsa moyo wace adzautaya: koma iye amene ataya moyo wace cifukwa ca Ine, adzaupeza.

26 Pakuti munthu adzapindulanji, akalandira dziko lonse, nataya moyo wace? kapena munthu adzaperekanji cosintha ndi moyo wace?

27 Pakuti Mwana wa munthu adzabwera mu ulemerero wa Atate wace, pamodzi ndi angelo ace; ndipo pomwepo Iye adzabwezera kwa anthu onse monga macitidwe ao.

28 Indetu ndinena kwa inu, kuti alipo ena a iwo aima pane sadzalawa ndithu imfa, kufikira adzaona Mwana wa munthu atadza mu ufumu wace.

17

1 Ndipo atapita masiku asanu ndi limodzi, Yesu anatenga Petro, ndi Yakobo, ndi Yohane mbale wace, napita nao pa okha pa phiri lalitari;

2 ndipo Iye anasandulika pamaso pao; ndipo nkhope yace inawala monga dzuwa, ndi zobvala zace zinakhala zoyera mbu monga kuwala.

3 Ndipo onani, Mose ndi Eliya anaonekera kwa iwo, alinkulankhula ndi Iye.

4 Ndipo Petro anayankha, nati kwa Yesu, Ambuye, kuli bwino kuti ife tikhale pano; ngati mulola ndidzamanga pane misasa itatu; umodzi wa Inu, ndi wina wa Mose, ndi wina wa Eliya.

5 Akali cilankhulire, onani, mtambo wowala unawaphi mba iwo: ndipo onani, mau alikunena mumtambo, Uyu ndiye Mwana wanga wokondedwa, mwa iyeyu ndikondwera, mverani Iye.

6 Ndipo pamene ophunzira anamva, anagwa nkhope zao pansi, naopa kwakukuru.

7 Ndipo Yesu anadza, nawakhudza nati, Ukani, musaopa,

8 Ndipo iwo, pokweza maso ao sanaona munthu, koma Yesu yekha.

9 Ndipo pamene anali kutsika paphiri, Yesu anawalangiza iwo kuti, Musakauze munthu coonekaco, kufikira Mwana wa munthu adadzauka kwa akufa.

10 Ndipo ophunzira ace anamfunsa, nanena, Ndipo bwanji alembi amanena kuti Eliya ndiye atsogole kudza?

11 Ndipo Iye anayankha, nati, Eliya akudzatu, nadzabwezera zinthu zonse;

12 koma ndinena kwa inu, kuti Eliya anadza kale, ndipo iwo sanamdziwa iye, koma anamcitira zonse zimene anazifuna iwo. Ndipo conconso Mwana wa munthu adzazunzidwa ndi iwo.

13 Pomwepo ophunzira anazindikira kuti analankhula nao za Yohane Mbatizi.

14 Ndipo pamene iwo anadza ku khamu la anthu, kunafika kwa Iye munthu, namgwadira Iye, nati,

15 Ambuye, citirani mwana wanga cifundo; cifukwa adwala khunyu, kuzunzika koipa: pakuti amagwa kawiri kawiri pamoto, ndi kawiri kawiri m'madzi.

16 Ndipo ndinadza naye kwa ophunzira anu, koma iwo sanathe kumciritsa.

17 Ndipo Yesu anayankha nati, Ha, obadwa osakhulupirira ndi amphulupulu, ndidzakhala ndi inu nthawi yanji? ndidzalekerera inu nthawi yanji? mudze naye kwa Ine kuno.

18 Ndipo. Yesu anamdzudzula; ndipo ciwanda cinaturuka mwa iye; ndipo mnyamatayo anacira kuyambira nthawi yomweyo.

19 Pamenepo ophunzira anadza kwa Yesu, ali pa yekha, nati, Nanga ife sitinakhoza bwanji kuciturutsa?

20 Ndipo Iye ananena kwa iwo, Cifukwa cikhulupiriro canu ncacing'ono: pakuti indetu ndinena kwa inu, Mukakhala naco cikhulupiriro monga kambeu kampiru, mudzati ndi phiri ili, Senderapo umuke kuja; ndipo lidzasendera; ndipo palibe kanthu kadzakulakani kosacitika. [

21 ]

22 Ndipo m'mene anali kutsotsa m'Galileya, Yesu ananena nao, Mwana wa munthu adzaperekedwa m'manja a anthu;

23 ndipo adzamupha Iye, ndipo Iye adzauka tsiku lacitatu. Ndipo iwo anali ndi cisoni cacikuru.

24 Ndipo pofika ku Kapernao arnene aja akulandira ndalama za kukacisi anadza kwa Petro nati, Kodi Mphunzitsi wanu sapereka rupiyalo?

25 Iye anabvomera, Apereka, Ndipo polowa iye m'nyumba, Yesu anatsogola kunena naye, nati, Simoni, uganiza bwanji? mafumu a dziko lapansi alandira msonkho kwa yani? kwa ana ao kodi, kapena kwa akunja?

26 Ndipo m'mene iye anati, Kwa akunja, Yesu ananena kwa iye, Cifukwa cace anawo ali aufulu.

27 Koma kuti ife tisawakhumudwitse, pita iwe kunyanja, ukaponye mbedza, nuitole nsomba yoyamba kuwedza; ndipo ukaikanula pakamwa pace udzapezamo rupiya; tatenga limeneli, nuwapatse ilo pamtu pa iwe ndi Ine.

18

1 Nthawi yomweyo ophunzira anadza kwa Yesu, nanena, Ndani kodi ali wopambana mu Ufumu wa Kumwamba?

2 Ndipo pamene Yesu anaitana kamwana, anakaimitsa pakati pao,

3 nati, Indetu ndinena kwa inu, Ngati simutembenuka, nimukhala monga tianato, simudzalowa konse mu Ufumu wa Kumwamba.

4 Cifukwa cace yense amene adzicepetsa yekha monga kamwana aka, yemweyo ali wopambana mu Ufumu wa Kumwamba.

5 Ndipo amene adzalandira kamwana kamodzi kotereka cifukwa ca dzina langa, alandira Ine;

6 koma yense amene adzakhumudwitsa kamodzi ka tiana iti, takukhulupirira Ine, kumuyenera iye kuti mphero yaikuru ikolowekedwe m'khosi mwace, namizidwe poya pa nyanja.

7 Tsoka liri hdi dziko lapansi cifukwa ca zokhumudwitsa! pakuti sikutheka kuti zokhumudwitsa zileke kudza, koma tsoka liri ndi munthu amene cokhumudwitsaco cidza ndi iye.

8 Ndipo ngati dzanja lako, kapena phazi lako likukhumudwitsa iwe, ulidule, nulitaye; nkwabwino, kuti ulowe m'moyo wopunduka dzanja kapena phazi, koposa kuponyedwa m'moto wa nthawi zonse, uli ndi manja awiri kapena mapazi awiri.

9 Ndipo ngati diso lako likukhumudwitsa, ulikolowole, nulitaye: nkwabwino kuti ulowe m'moyo ndi diso limodzi koposa kuponyedwa m'gehena wamoto, uli ndi maso awiri.

10 Yang'anirani kuti musanyoze mmodzi wa ang'ono awa; pakuti ndinena kwa inu, kuti angelo ao apenya cipenyere nkhope ya Atate wanga wa Kumwamba. [

11 ]

12 Nanga muyesa bwanji? ngati munthu ali nazo nkhosa makumi khumi, ndipo ikasokera imodzi ya izo, kodi saleka zija makumi asanu ndi anai mphambu manu ndi zinai, napita kumapiri, kukafuna yosokerayo?

13 Ndimo akaipeza, indedi ndinena kwa inu, akondwera nayo koposa ndi makumi asanu ndi anai mphambu zisanu ndi zinai zosasokera.

14 Comweco siciri cifuniro ca Atate wanu wa Kumwamba kuti mmodzi wa ang'ono awa atayike.

15 Ndipo ngati mbale wako akucimwira iwe, pita, numlangize pa nokha iwe ndi iye; ngati akumvera iwe, wambweza mbale wako.

16 Koma ngati samvera, onjeza kutenga ndi iwe wina mmodzi kapena awiri, kuti atsimikizidwe mau onse pakamwa pa mboni ziwiri kapena zitatu.

17 Ndipo ngati iye samvera iwo, uuze Mpingo; ndipo ngati iye samveranso Mpingowo, akhale kwa iwe monga wakunja ndi wamsonkho.

18 Indetu ndinena kwa inu, Ziri zonse mukazimanga pa dziko lapansi zidzakhala zomangidwa Kumwamba: ndipo ziri zonse mukazimasula pa dziko lapansi, zidzakhala zomasulidwa Kumwamba.

19 Ndiponso ndinena kwa inu kuti ngati awiri ainu abvomerezana pansi pano cinthu ciri conse akacipempha, Atate wanga wa Kumwamba adzawacitira.

20 Pakuti kumene kuli awiri kapena atatu asonkhanira m'dzina langa, ndiri komweko pakati pao.

21 Pamenepo Petro anadza, nati kwa Iye, Ambuye, mbale wanga adzandilakwira kangati, ndipo ine ndidzamkhululukira iye? kufikira kasanu ndi kawiri kodi?

22 Yesu ananena kwa iye, Sindinena kwa iwe kufikira kasanu ndi kawiri, koma kufikira makumi ananu ndi awiri kubwerezedwa kasanu ndi kawiri.

23 Cifukwa cace Ufumu wa Kumwamba ufanizidwa ndi munthu, mfumu, amene anafuna kuwerengera nao akapolo ace.

24 Ndipo pamene anayamba kuwerengera, anadza kwa iye ndi wina wamangawa wa ndalama za matalente zikwi khumi.

25 Koma popeza iye anasowa kanthu kombwezera, mbuye wace analamulira kuti iye agulitsidwe, ndi mkazi wace ndi ana ace omwe, ndi zonse ali nazo, kuti akabwezedwe mangawawo.

26 Cifukwa cace kapoloyo anagwadapansi, nampembedzera, nati, Mbuye, bakandiyembekezani ine, ndipo zonse ndidzazibwezera kwa inu.

27 Ndipo mbuye wa kapoloyo anagwidwa ndi cisoni mumtima, nammasula iye, namkhululukira ngongole.

28 Koma kapolo uyu, poturuka anapeza wina wa akapolo anzace yemwe anamkongola iye marupiya atheka makumi khumi, namgwira, namkanyanga pakhosi, nati, Bwezera cija unacikongola.

29 Pamenepo kapolo mnzaceyu anagwada pansi, nampempha iye, nati, Bakandiyembekeza ine, ndipo ndidzakubwezera.

30 Ndipo iye sanafuna; koma anamuka, namponya iye m'nyumba yandende, kufikira abwezere ngongole.

31 Cifukwa cace m'mene akapolo anzace anaona zocitidwazo, anagwidwa cisoni cacikuru, nadza, nalongosolera mbuye wao zonse zimene zinacitidwa.

32 Pomwepo mbuye wace anamuitana iye, nanena naye, Kapolo iwe weipa, ndinakukhululukira iwe mangawa onse aja momwe muja unandipempha ine;

33 kodi iwenso sukadamcitira kapolo mnzako cisoni, monga inenso ndinakucitira iwe cisoni?

34 Ndipo mbuye wace anakwiya, nampereka kwa azunzi, kufikira akambwezere iye mangawa onse.

35 Comweconso Atate wanga adzacitira inu, ngati inu simukhululukira yense mbale wace ndi mitima yanu.

19

1 Ndipo panali pamene Yesu anatha mau amenewa, anacokera ku Galileya, nadza ku malire a Yudeya, a ku tsidya lija la Yordano.

2 Ndipo makamu akuru a anthu anamtsata; ndipo Iye anawaciritsa kumeneko.

3 Ndipo Afarisi anadza kwa Iye, namuyesa, nanena, Kodi nkuloledwa kuti munthu acotse mkazi wace pa cifukwa ciri conse?

4 Ndipo Iye anayankha, nati, Kodi simunawerenga kuti Iye amene adalenga anthu paciyambi, anawalenga iwo mwamuna ndi mkazi,

5 nati, Cifukwa ca ici mwamuna adzasiya atate wace ndi amace, nadzaphatikizana ndi mkazi wace, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi?

6 cotero kuti salinso awiri koma thupi limodzi. Cifukwa cace ici cimene Mulungu anacimanga pamodzi, munthu asacilekanitse.

7 Iwo ananena kwa Iye, Nanga cifukwa ninji Mose analamulira kupatsa kalata wa cilekaniro, ndi kumcotsa?

8 Iye ananena kwa iwo, Cifukwa ca kuuma mtima kwanu, Mose anakulolezani kucotsa akazi anu; koma paciyambi sikunakhala comweco.

9 Ndipo Ine ndinena kwa inu, Amene ali yense akacotsa mkazi wace, kosakhala cifukwa ca cigololo, nadzakwatira wina, acita cigololo: ndipo iye amene akwatira wocotsedwayo, acita cigololo.

10 Ophunzira ananena kwa Iye, Ngati mlandu wa munthu ndi mkazi wace uti wotere, sikuli kwabwino kukwatira.

11 Koma Iye anati kwa iwo, Onse sangathe kulandira conena ici, koma kwa iwo omwe capatsidwa.

12 Pakuti pali osabala, amene anabadwa otero m'mimba ya amao: ndipo pali osabala anawafula anthu; ndipo pali osabala amene anadzifula okha, cifukwa ca Ufumu wa Kumwamba. Amene angathe kulandira ici acilandire.

13 Pamenepo anadza nato tiana kwa Iye, kuti Iye aike manja ace pa ito, ndi kupemphera: koma ophunzirawo anawadzudzula.

14 Koma Yesu anati, Tilekeni tiana, musatikanize kudza kwa Ine: cifukwa Ufumu wa Kumwamba uli wa totere.

15 Ndipo Iye anaika manja ace pa ito, nacokapo.

16 Ndipo onani, munthu anadza kwa Iye, nati, Mphunzitsi, cabwino nciti ndicicite, kuti ndikhale nao mayo wosatha?

17 Ndipo Iye anati kwa iye, Undifunsiranji za cinthu cabwino? alipo Mmodzi ndiye wabwino: koma ngati ufuna kulowa m'moyo, sunga malamulo.

18 Iye ananena kwa Iye, Otani? Ndipo Yesu anati, Usaphe, Usacite cigololo, Usabe, Usacite umboni wonama,

19 Lemekeza atate wako ndi amako, ndipo, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.

20 Mnyamatayo ananena kwa Iye, Zonsezi ndinazisunga, ndisowanso ciani?

21 Yesu ananena naye, Ngati ufuna kukhala wangwiro, pita, kagulitse zomwe uli nazo, nupatse aumphawi, ndipo udzakhaia ndi cuma Kumwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate.

22 Koma mnyamatayo m'mene anamva conenaco, anamuka wacisoni; pakuti anali naco cuma cambiri.

23 Ndipo Yesu anati kwa ophunzira ace, Indetu ndinena kwa inu, kuti munthu mwini cuma adzalowa mobvutika mu Ufumu wa Kumwamba.

24 Ndiponso ndinena kwa inu, Nkwapafupi kuti ngamila ipyole diso la singano, koposa mwini cuma kulowa Ufumu wa Kumwamba.

25 Ndipo ophunzira, pamene anamva, anazizwa kwambiri, nanena, Ngati nkutero angapulumuke ndani?

26 Ndipo Yesu anawayang'ana, nati kwa iwo, ici sicitheka ndi anthu, koma zinthu zonse zitheka ndi Mulungu.

27 Pomwepo Petro anayankha, nati kwa Iye, Onani, ife tinasiya zonse ndi kutsata Inu; nanga tsono tidzakhala ndi ciani?

28 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Indetu ndinena kwa inu, kuti inu amene munanditsata Ine, m'kubadwanso, pamene Mwana wa munthu adzakhala pa cimpando ca ulemerero wace, inunso, mudzakhala pa mipando khumi ndi iwiri, kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israyeli.

29 Ndipo onse amene adasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena atate, kapena amai, kapena ana, kapena minda, cifukwa ca dzina langa, adzalandira zobwezeredwa zambirimbiri, nadzalowa moyo wosatha.

30 Koma ambiri oyamba adzakhala akuthungo, ndi akuthungo adzakhala oyamba.

20

1 Pakuti Ufumu wa Kumwamba ufanana ndi munthu mwini banja, amene anaturuka mamawa kuka lembera anchito a m'munda wace wampesa.

2 Ndipo parnene adapangana ndi anchito, pa rupiya latheka limodzi tsiku limodzi, anawatumiza ku munda wace.

3 Ndipo anaturuka dzuwa litakwera, naona ena ataima cabe pabwalo;

4 ndipo kwa iwo anati, Pitani inunso kumunda, ndipo ndidzakupatsani cimene ciri coyenera. Ndipo iwo anapita.

5 Ndiponso anaturuka usana, ndimonso popendeka dzuwa, nacita cimodzimodzi.

6 Ndipo poyandikira madzulo anaturuka, napeza ena ataima; nanena kwa iwo, Mwaimiranji kuno dzuwa lonse cabe?

7 Iwo ananena kwa iye, Cifukwa palibe munthu anatilemba. Iye anati kwa iwo, Pitani inunso ku mundawo wampesa.

8 Ndipo pamadzulo, mwini munda anati kwa kapitao wace, Kaitane anchito, nuwapatse iwo kulipira kwao, uyambe kwa omarizira kufikira kwa oyamba.

9 Ndipo pamene iwo olembedwa poyandikira madzulo anadza, analandira munthu ali yense rupiya latheka limodzi.

10 Ndipo m'mene oyamba anadza, analingalira kuti adzalandira kopambana, ndipo iwonso analandira onse rupiya latheka.

11 Koma m'mene iwo analilandira, anaderera kwa mwini banja,

12 nati, Omarizira awa anagwira nchito mphindi yaing'ono, ndipo munawalinganiza ndi ife amene tinapirira kuwawa kwa dzuwa ndi: kutentha kwace.

13 Koma iye anayankha, nati kwa mmodzi wa iwo, Mnzanga, sindikunyenga iwe; kodi iwe sunapangana ndi ine pa rupiya latheka limodzi?

14 Tenga lako, numuke; pakuti ine ndifuna kupatsa kwa uyu womarizira monga kwa iwe.

15 Sikuloleka kwa ine kodi kucita cimene ndifuna ndi zanga? Kapena diso lako laipa kodi cifukwa ine ndiri wabwino?

16 Comweco omarizira adzakhala oyamba, ndipo oyamba adzakhala omarizira.

17 Ndipo pamene Yesu analikukwera ku Yerusalemu, anatenga ophunzira khurni ndi awiri napita nao pa okha, ndipo panjira anati kwa iwo,

18 Onani, tikwera ku Yerusalemu; ndipo Mwana wa munthu adzaperekedwa kwa ansembe akuru ndi alembi, ndipo iwo adzamweruza kuti ayenera imfa,

19 nadzampereka kwa anthu akunja kuti amnyoze ndi kumkwapula, ndi kumpacika; ndipo Iye adzaukitsidwa tsiku lacitatu.

20 Pomwepo anadza kwa Iye amace a ana a Zebedayo ndi ana ace omwe, namgwadira, ndi kumpempha kanthu.

21 Ndipo Iye anati kwa iye, Ufuna ciani? Iye ananena, Lamulirani kuti ana anga awiri amenewa adzakhale, wina ku dzanja lanu lao manja, ndi wina kulamanzere, mu ufumu wanu.

22 Koma Yesu anayankha nati, Inu simudziwa cimene mupempha, Kodi mukhoza kumwera cikho nditi ndidzamwere Ine? Iwo ananena kwa Iye, Ife tikhoza.

23 Iye ananena kwa iwo, Cikho canga mudzamweradi; koma kukhala ku dzanja lamanja kwangandi kulamanzere, sikuli kwanga kupatsa, koma kuli kwa iwo omwe kwakonzedweratu ndi Atate wanga.

24 Ndipo m'mene khurniwo anamva, anapsa mtima ndi abale awiriwo.

25 Koma Yesu anawaitana, nati, Mudziwa kuti mafumu a anthu amadziyesa okha ambuye ao, ndipo akuru ao amacita ufumu pa iwo.

26 Sikudzakhala comweco kwa inu ai; koma amene ali yense akafuna kukhala warnkuru mwa inu, adzakhala mtumiki wanu;

27 ndipo amene ali yense akafuna kukhala woyamba mwa inu, adzakhala kapolo wanu:

28 monga Mwana wa munthu sanadza kutumikiridwa koma kutumikira, ndi kupereka moyo wace dipo la anthu ambiri.

29 Ndipo pamene iwo analikuturuka m'Yeriko, khamu lalikuru la anthu linamtsata Iye.

30 Ndipo onani, anthu akhungu awiri anakhala m'rnphepete mwa njira; m'mene iwo anamva kuti Yesu analikupitirirapo, anapfuula nati, Muticitire ife cifundo, Inu Mwana wa Davide.

31 Ndipo khamulo linawaletsa, kuti atonthole: koma anakuwitsa, nanena, Ambuye, muticitire cifundo, Inu Mwana wa Davide.

32 Ndipo Yesu anaima, nawaitana, nati, Mufuna kuti ndikucitireni ciani?

33 Ananena kwa Iye, Ambuye, kuti maso athu apenye,

34 Ndipo Yesu anagwidwa ndi cifundo, nakhudza maso ao; ndipo pornwepo anapenyanso, namtsata Iye.

21

1 Ndipo parnene iwo anayandikira ku Yerusalemu, nafika ku Betefage, ku phiri la Azitona, pamenepo Yesu anatumiza ophunzira awiri,

2 nanena kwa iwo, Mukani ku mudzi wopenyana ndi inu, ndipo pomwepo mudzapeza buru womangidwa, ndi mwana wace pamodzi nave, masulani iwo, mudze nao kwa Ine.

3 Ndipo munthu akanena kanthu ndi inu, mudzati, Ambuye asowa iwo, Ndipo pomwepo adzawatumiza.

4 Ndipo ici cinatero, kuti cikacitidwe conenedwa ndi mneneri kuti,

5 Tauzani mwanawamkazi wa Ziyoni, Taona, Mfumu yako idza kwa iwe, Wofatsa ndi wokwera pa buru, Ndi pa kaburu, mwana wa nyama yonyarnula katundu.

6 Ndipo ophunzirawo anamuka, nacita monga Yesu anawauza;

7 nabwera ndi buru ndi mwana wace, naika pa iwo zobvala zao, nakhala Iye pamenepo.

8 Ndipo ambirimbiri a mpingowo anayala zobvala zao panjira; Ndipo ena anadula nthambi za mitengo, naziyala m'njirarno.

9 Ndipo mipingo yakumtsogolera ndi yakumtsatira, inapfuula, kuti, Hosana kwa Mwana wa Davide! Wolemekezeka ndiye wakudza m'dzina la Ambuye! Hosana m'Kumwambamwamba!

10 Ndipo m'mene adalowa m'Yerusalemu mudzi wonse unasokonezeka, nanena, ndani uyu?

11 Ndipo makamu a anthu anati, Uyu ndi mneneri Yesu wa ku Nazarete wa ku Galileya.

12 Ndipo Yesu analowa ku Kacisi wa Mulungu naturutsira kunja onse akugulitsa ndi kugula malonda, nagubuduza magome a osintha ndalama, ndi mipando ya ogulitsa nkhunda;

13 nanena kwa iwo, Calembedwa, Nyumba yanga idzanenedwa nyumba yakupemphera; koma inu mwaiyesa phanga la acifwamba.

14 Ndipo anadza kwa Iye kuKacisiko akhungu ndi opunduka miyendo, naciritsidwa.

15 Koma ansembe akuru ndi alembi, m'mene anaona zozizwitsa zomwe Iye anazicita, ndi ana alinkupfuula kuKacisiko kuti, Hosana kwa Mwana wa Davide, anapsa mtima,

16 nanena kwa Iye, Mulinkumva kodi cimene alikunena awa? Ndipo Yesu ananena kwa iwo, Inde: simunawerenga kodi, M'kamwa mwa makanda ndi oyamwa munafotokozera zolemekeza?

17 Ndipo Iye anawasiya, naturuka m'mzinda, napita ku Betaniya, nagona kumeneko.

18 Ndipo mamawa, m'mene Iye analinkunkanso kumzinda, anamva njala,

19 Ndipo pakuona mkuyu umodzi panjira, anafika pamenepo, napeza palibe kanthu koma masamba okha okha; nati Iye kwa uwo, Sudzabalanso cipatso ku nthawi zonse. Ndipo pomwepo mkuyuwo unafota.

20 Ndipo ophunzira poona ici anazizwa, nati, Mkuyuwo unafota bwanji msanga?

21 Ndipo Yesu anayankha, nati kwa iwo, Indedi ndinena kwa inu, Ngati mukhala naco cikhulupiriro, osakayika-kayika, mudzacita si ici ca pa mkuyu cokha, koma ngati mudzati ngakhale ku phiri ili, Tanyamulidwa, nuponyedwe m'nvania, cidzacitidwa.

22 Ndipo zinthu ziri zonse mukazifunsa m'kupemphera ndi kukhulupirira, mudzazilandira.

23 Ndipo m'mene Iye analowa m'Kacisi, ansembe akuru ndi akuru anthu anadza kwa Iye analikuphunzitsa, nanena, Mucita izi ndi ulamuliro wotani? Ndipo ndani anakupatsani ulamuliro wotere?

24 Ndipo Yesu anayankha, nati kwa iwo, Inenso ndikufunsani mau amodzi, amene ngati muneliuza, Inenso ndikuuzani ndi ulamuliro wotani ndizicita izi:

25 Ubatizo wa Yohane, ucokera kuti? Kumwamba kodi kapena kwa anthu? Koma iwo anafunsana wina ndi mnzace, kuti, Tikati, Kumwamba, Iye adzati kwa ife, Munalekeranji kumvera iye?

26 Koma tikati, Kwa anthu, tiopa khamulo la anthu; pakuti onse amuyesa Yohane mneneri.

27 Ndipo anamyankha Yesu, nati, Sitidziwa ife. Iyenso ananena nao, lnenso sindikuuzani ndi ulamuliro wotani ndizicita izi.

28 Nanga mutani? Munthu anali cao ana awiri; nadza iye kwa woyamba nati, Mwanawe, kagwire lero nchito ku munda wampesa.

29 Koma iye anakana, nati, Sindifuna ine; koma pambuyo pace analapa mtima napita.

30 Ndipo anadza kwa winayo, natero momwemo. Ndipo iye anabvomera, nati, Ndipita mbuye; koma sanapita.

31 Ndani wa awiriwo anacita cifuniro ca atate wace? Iwo ananena, Woyambayo. Yesu ananena kwa iwo, Indetu ndinena kwa inu, kuti amisonkho ndi akazi aciwerewere amatsogolera inu, kulowa mu Ufumu wa Kumwamba.

32 Popeza Yohane anadza kwa inu m'njira ya cilungamo, ndipo simunamveraiye; koma amisonkho ndi akazi aciwerewere anammvera iye; ndipo inu, m'mene munaciona, simunalapa pambuyo pace, kuti mumvere iye.

33 Mverani fanizo lina: Panali munthu, mwini banja, amene analima munda wamphesa, nauzunguniza linga, nakumba umo moponderamo mphesa, namanga nsanja, naukongoletsa kwa olima munda, namuka kwina.

34 Ndipo pamene nyengo ya zipatso inayandikira, anatumiza akapolo ace kwa olima mundawo, kukalandira zipatso zace.

35 Ndipo olimawo anatenga akapolo ace, nampanda mmodzi, wina namupha, wina namponya miyala.

36 Anatumizanso akapolo ena, akucuruka oposa akuyambawa; ndipo anawacitira iwo momwemo.

37 Koma pambuyo pace anatumiza kwa iwo mwana wace, nati, Adzacitira mwana wanga ulemu.

38 Koma olimawo m'mene anaona mwanayo, ananena wina ndi mnzace, Uyo ndiye wolowa; tiyeni, timuphe, ndipo ife tidzatenga colowa cace.

39 Ndipo anamtenga iye, namponya kunja kwa munda, namupha.

40 Tsono atabwera mwini munda, adzacitira olimawo ciani?

41 Iwo ananena kwa Iye, Adzaononga koipa oipawo, nadzapereka mundawo kwa olima ena, amene adzambwezera iye zipatso pa nyengo zace.

42 Yesu ananena kwa iwo, 1 Kodi simunawerenga konse m'malembo, Mwala umene anaukana omanga nyumba Womwewu unakhala mutu wa pangondya: ici cinacokera kwa Ambuye, Ndipo ciri cozizwitsa m'maso mwathu?

43 Cifukwa cace ndinena kwa inu, 2 Ufumu wa Mulungu udzacotsedwa kwa inu, nudzapatsidwa kwa anthu akupatsa zipatso zace.

44 Ndipo 3 iye wakugwa pa mwala uwu adzaphwanyika; koma pa iye amene udzamgwera, udzampera iye.

45 Ndipo ansembe akuru ndi Afarisi, pakumva mafanizo ace, anazindikira kuti alikunena za iwo.

46 Ndipo pamene anafuna kumgwira, anaopa makamu a anthu, 4 cifukwa anamuyesa mneneri.

22

1 Ndipo Yesn anayankha, nalankhulanso kwa iwo m'mafanizo, nati,

2 Ufumu wa Kumwamba ufanafana ndi munthu, mfumu, amene anakonzera mwana wace phwando la ukwati,

3 natumiza akapolo ace kukaitana oitanidwa ku ukwati umene; ndipo iwo sanafuna kudza.

4 Pomwepo anatumizanso akapolo ena, nanena, Uzani oitanidwawo, Onani, ndakonza phwando langa; ng'ombe zanga, ndi zonona ndinazipha, ndi zinthu zonse zapsya: idzani kuukwati.

5 Koma iwo ananyalanyaza, nacoka, wina ku munda wace, wina ku malonda ace:

6 ndipo otsala anagwira akapolo ace, nawacitira cipongwe, nawapha.

7 Koma mfumu inakwiya; nituma asilikari ace napululutsa ambanda aja, nitentha mudzi wao.

8 Pomwepo inanena kwa akapolo ace, Za ukwati tsopano zapsya, koma oitanidwawo sanayenera.

9 Cifukwa cace pitani inu ku mphambano za njira, ndipo amene ali yense mukampeze, itanani kuukwatiku.

10 Ndipo akapolo ao anaturukira kunjira, nasonkhanitsa onse amene anawapeza, ngakhale oipa, ngakhale abwino; ndipo ukwatiwo unadzala ndi okhala pacakudya.

11 Koma mfumuyo m'mene inadza kuwaona akudyawo, anapenya momwemo munthu wosabvala cobvala ca ukwati;

12 nanena kwa iye, Mnzangawe, unalowa muno bwanji wosakhala naco cobvala ca ukwati? Ndipo iye analibe mau.

13 Pomwepo mfumu inati kwa atumiki, Mumange iye manja ndi miyendo, mumponye ku mdima wakunja; komweko kudzali kulira ndi kukukuta mano.

14 Pakuti oitanidwa ndiwo ambiri, koma osankhidwa ndiwo owerengeka.

15 Pomwepo Afarisi anamuka, nakhala upo wakumkola Iye m'kulankhula kwace.

16 Ndipo anatumiza kwa Iye ophunzira ao, pamodzi ndi Aherode, amene ananena, Mphunzitsi, tidziwa kuti muli woona, ndipo muphunzitsa njira ya Mulungu moona ndithu, ndipo simusamala munthu ali yense; pakuti simuyang'anira pa nkhope ya anthu.

17 Cifuka cace mutiuze ife, muganiza ciani? Kuloledwa kodi kupatsa msonkho kwa Kaisara, kapena iai?

18 Koma Yesu anadziwa kuipa kwao, nati, Mundiyeseranji Ine, onyenga inu?

19 Tandionetsani Ine ndalama yamsonkho. Ndipo iwo anadza nalo kwa Iye rupiya latheka.

20 Ndipo Iye anati kwa iwo, Nca yani cithunzithunzi ici, ndi kulemba kwace?

21 Nanena iwo, Ca Kaisara. Pomwepo Iye anati kwa iwo, Cifukwa cace patsani kwa Kaisara zace za Kaisara, ndi kwa Mulungu zace za Mulungu.

22 Ndipo pamene iwo anamva, anazizwa, namsiya Iye, nacokapo.

23 Tsiku lomwelo anadza kwa Iye Asaduki, amene amanena kuti palibe kuuka kwa akufa; namfunsa Iye,

24 nanena, Mphunzitsi, Mose anati, Ngati munthu akafa wopanda mwana, mphwace adzakwatira mkazi wace, nadzamuukitsira mbale wace mbeu.

25 Tsono panali ndi ife abale asanu ndi awiri; ndipo wakuyamba anakwatira, namwalira wopanda mbeu, nasiyira mphwace mkazi wace;

26 cimodzimodzi waciwiri, ndi wacitatu, kufikira wacisanu ndi ciwiri.

27 Ndipo pomarizira anamwaliranso mkaziyo.

28 Cifukwa cace m'kuuka kwa akufa, iye adzakhala mkazi wa yani wa asanu ndi awiriwo? pakuti onse anakhala naye.

29 Koma Yesu anayankha, nati kwa iwo, Mungolakwa a osadziwa malembo, kapena mphamvu za Mulungu.

30 Pakuti m'kuuka kwa akufa sakwatira, kapena kukwatiwa, koma akhala ngati angelo a Kumwamba.

31 Koma za kuuka kwa akufa, simunawerenga kodi comwe cinanenedwa kwa inu ndi Mulungu, kuti,

32 Ine ndiri Mulungu wa Abrahamu, ndi Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo? Sali Mulungu wa akufa koma wa amoyo.

33 Ndipo pamene makamu a anthu anamva, anazizwa ndi ciphunzitso cace.

34 Koma Afarisi, pakumva kuti Iye anatontholetsa Asaduki, anasonkhana.

35 Ndipo mmodzi wa iwo, mphunzitsi wa cilamulo, anamfunsa ndi kumuyesa Iye, nati,

36 Mphunzitsi, lamulo lalikuru ndi liti la m'cilamulo?

37 Ndipo Yesu anati kwa iye, Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse.

38 Ili ndilo lamulo lalikuru ndi loyamba.

39 Ndipo laciwiri lolingana nalo ndili, Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.

40 Pa malamulo awa awiri mpokolowekapo cilamulo conse ndi aneneri.

41 Ndipo pamene Afarisi anasonkhana, Yesu anawafunsa,

42 nati, Muganiza bwanji za Kristu? ali mwana wa yani? Iwo ananena kwa Iye, Wa Davide.

43 Iye anati kwa iwo, Ndipo Davide mu Mzimu amchula Iye bwanji Ambuye, nanena,

44 Ambuye ananena kwa Ambuye wanga, Ukhale pa dzanja lamanja langa, Kufikira Ine ndidzaika adani ako pansi pa mapazi ako.

45 Cifukwa cace ngati Davide amchula Iye Ambuye, ali mwana wace bwanji? Ndipo panalibe mmodzi anatha kumyankha mau.

46 Ndipo sanalimbika mtima munthu ali yense kumfunsa kanthu kuyambira tsiku lomwelo.

23

1 Pomwepo Yesu analankhula ndi makamu a anthu ndi ophunzira ace,

2 nanena, Alembi ndi Afarisi akhala pa mpando wa Mose;

3 cifukwa cace zinthu ziri zonse zimene iwo akauza inu, citani nimusunge; koma musatsanza nchito zao; pakuti iwo amalankhula, komasamacita.

4 Inde, amanga akatundu olemera ndi osautsa ponyamula, nawasenza pa mapewa a anthu; koma iwo eni okha safuna kuwasuntha amenewo ndi cala cao.

5 Koma amacita nchito zao zonse kuti aonekere kwa anthu; pakuti akulitsa citando cace ca njirisi zao, nakulitsa mphonje,

6 nakonda malo a ulemu pamapwando, ndi mipando ya ulemu m'masunagoge,

7 ndi kulankhulidwa m'misika, ndi kuchedwa ndi anthu, Rabi.

8 Koma inu musachedwa Rabi; pakuti Mphunzitsi wanu ali mmodzi, ndipo inu nonse muli abale.

9 Ndipo inu musachule wina atate wanu pansi pano, pakuti alipo mmodzi ndiye Atate wanu wa Kumwamba.

10 Ndipo musachedwa atsogoleri, pakuti alipo mmodzi Mtsogoleri wanu, ndiye Kristu.

11 Koma wamkuru wopambana wa inu adzakhala mtumiki wanu.

12 Ndipo amene ali yense akadzikuza yekha adzacepetsedwa; koma amene adzicepetsa mwini yekha adzakulitsidwa.

13 Koma tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! cifukwa mutsekera anthu Ufumu wa Kumwamba pamaso pao; pakuti inu nokha simulowamo, Ndipo muwaletsa amene alikulowa, kuti asalowemo. [

14 ]

15 Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! cifukwa mupitapita kunyanja ndi kumtunda kuyesa munthu mmodzi mtembenuki; ndipo m'mene akhala wotere, mumsandutsa mwana wa gehena woposa inu kawiri.

16 Tsoka inu, atsogoleri akhungu, amene munena, Amene ali yense akalumbira kuchula Kacisi, palibe kanthu; koma amene akalumbira kuchula golidi wa Kacisi, wadzimangirira.

17 Inu opusa, ndi akhungu: pakuti coposa nciti, golidi kodi, kapena Kacisi amene ayeretsa golidiyo?

18 Ndiponso, Amene ali yense akalumbira kuchula guwa la nsembe, palibe kanthu; koma amene akalumbira kuchula mtulo wa pamwamba pace wadzimangirira.

19 Inu akhungu, pakuti coposa nciti, mtulo kodi, kapena guwa la nsembe limene liyeretsa mtulowo?

20 Cifukwa cace wakulumbira kuchula guwa la nsembe, alumbira limenelo ndi zonse za pamwamba pace.

21 Ndipo wakulumbira kuchula Kacisi, alumbira ameneyo ndi Iye wakukhala momwemo.

22 Ndipo wakulumbira kuchula Kumwamba, alumbira cimpando ca Mulungu, ndi Iye wakukhala pomwepo.

23 Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! cifukwa mupereka limodzi la magawo khumi la timbeu tonunkhira, ndi katsabola, ndi la citowe, nimusiya zolemera za cilamulo, ndizo kuweruza kolungama, ndi kucitira cifundo, ndi cikhulupiriro; koma zijazo munayenera kuzicita, osasiya izi zomwe.

24 Atsogoleri akhungu inu, akukuntha udzudzu, koma ngamila mummeza.

25 Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! cifukwa mutsuka kunja kwace kwa cikho ndi mbale, koma m'katimo iwo adzala ndi kulanda ndi kusadziletsa.

26 Mfarisi iwe wakhungu, yambotsuka m'kati mwa cikho ndi mbale, kuti kunja kwace kukhalenso koyera.

27 Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! cifukwa mufanafana ndi manda opaka njereza, amene aonekera okoma kunja kwace, koma adzala m'katimo ndi mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zonse.

28 Comweco inunso muonekera olungama pamaso pa anthu, koma m'kati muli odzala ndi cinyengo ndi kusayeruzika.

29 Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! cifukwa mumanga nyumba za pa manda a aneneri, ndipo mukonza manda a anthu olungama,

30 ndi kuti, Ife tikadakhala m'masiku a makolo anthu, sitikadakhala oyanjana nao pa mwazi wa aneneri.

31 Pomwepo mutsimikiza nokha, kuti muli ana a iwo amene anapha aneneri.

32 Dzazani inu muyeso wa makolo anu.

33 Njoka inu, obadwa inu a mamba, mudzatha bwanji kuthawa kulanga kwace kwa gehena?

34 Cifukwa ca ici, onani, ndituma kwa inu aneneri ndi anzeru ndi alembi; ena a iwo mudzawapha, mudzawapacika; ndi ena a iwo mudzawakwapula m'masunagoge mwanu, ndi kuwazunza, kucokera ku mudzi umodzi, kufikira ku mudzi wina;

35 kotero kuti udzafika pa inu mwazi wonse wotayidwa pa dziko lapansi, kuyambira ku mwazi wa Abele wolungamayo, kufikira ku mwazi wa Zakariya mwana wa Barakiya, amene munamupha pakati pa Kacisi ndi guwa la nsembe.

36 Indetu ndinena kwa inu, Zinthu zonse izi zidzafika pa mbadwo uwu wamakono.

37 Ha, Yerusalemu, Yerusalemu, amene umapha aneneri, ndi kuwaponya miyala iwo otumidwa kwa iwe! Ine ndinafuna kangati kusonkhanitsa pamodzi ana ako, inde monga thadzi lisonkhanitsa anapiye ace m'mapiko ace, koma inu simunafuna ai!

38 Onani, nyumba yanu yasiyidwa kwa inu yabwinja.

39 Pakuti ndinena kwa inu, Simudzandionanso Ine, kuyambira tsopano, kufikira mudzanena, Wolemekezedwa Iye amene akudza m'dzina la Ambuye.

24

1 Ndipo Yesu anaturuka kuKacisi; ndipo ophunzira ace anadza kudzamuonetsa cimangidwe ca Kacisiyo.

2 Koma Iye anayankha nati kwa iwo, Simuona izi zonse kodi? indetu ndinena kwa inu, Sipadzakhala pano mwala umodzi pa unzace, umene sudzagwetsedwa.

3 Ndipo pamene Iye analikukhala pansi pa phiri la Azitona, ophunzira anadza kwa Iye pa yekha, nanena, Mutiuze ife zija zidzaoneka liti? ndipo cizindikiro ca kufika kwanu nciani, ndi ca mathedwe a nthawi ya pansi pano?

4 Ndipo Yesu anayankha nati kwa iwo, Yang'anirani, asasokeretse inu munthu.

5 Pakuti ambiri adzafika m'dzina langa, nadzanena, Ine ndine Kristu, nadzasokeretsa anthu ambiri.

6 Koma inu mudzayamba kumva za nkhondo, ndi mbiri za nkhondo; onani, musadere nkhawa; pakuti kuyenera kuti izi zioneke; koma citsiriziro sicinafike.

7 Pakuti mtundu umodzi wa anthu udzaukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu ndi ufumu wina; ndipo kudzakhala njala ndi zibvomezi m'malo akuti akuti.

8 Koma ndizo zonsezi zowawa zoyamba.

9 Pamenepo adzakuperekani kunsautso, nadzakuphani; ndipo anthu a mitundu yonse adzadana nanu, cifukwa ca dzina langa.

10 Ndipo pomwepo ambiri adzakhumudwa, nadzaperekana wina ndi mnzace, nadzadana wina ndi mnzace.

11 Ndipo aneneri onama ambiri adzauka, nadzasokeretsaanthuambiri.

12 Ndipo cifukwa ca kucuruka kwa kusayeruzika, cikondano ca anthu aunyinji cidzazirala.

13 Koma iye wakulimbika cilimbikire kufikira kucimariziro, yemweyo adzapulumuka.

14 Ndipo uthenga uwu wabwino wa Ufumu udzalalikidwa pa dziko lonse lapansi, ukhale mboni kwa anthu h mitundu yonse; ndipo pomwepo cidzafika cimariziro.

15 Cifukwa cace m'mene mukadzaona conyansa ca kupululutsa, cimene cidanenedwa ndi Danieli mneneri, citaima m'malo oyera (iye amene awerenga m'kalata azindikire)

16 pomwepo iwo ali m'Yudeya athawire kumapiri:

17 iye ali pamwamba pa chindwi, asatsikire kunyamula za m'nyumba mwace;

18 ndi iye wa m'munda asabwere kutenga copfunda cace.

19 Koma tsoka ali nalo iwo akukhala ndi pakati, ndi akuyamwitsa ana m'masiku awo!

20 Ndipo pempherani kuti kuthawa kwanu kusakhale pa nyengo yacisanu, kapena pa Sabata;

21 pakuti pomwepo padzakhala masauko akuru, monga sipadakhale otero kuyambira ciyambi ca dziko, kufikira tsopano, inde ndipo sipadzakhalanso.

22 Ndipo akadaleka kufupikitsidwa masiku awo, sakadapulumuka munthu ali yense: koma cifukwa ca osankhidwawo masiku awo adzafupikitsidwa.

23 Pomwepo munthu akanena kwa inu, Onani, Kristu ali kuno, kapena uko musambvomereze;

24 cifukwa Akristu onama adzauka, ndi aneneri onama nadzaonetsa zizindikiro zazikuru ndi zozizwa: kotero kuti akanyenge, ngati nkotheka, osankhidwa omwe. Onani ndakuuziranitu pasadafike.

25 Cifukwa cace akanena kwa inu, Onani, Iye ali m'cipululu; musamukeko.

26 Onani, ali m'zipinda; musabvomereze.

27 Pakuti monga mphezi idzera kum'mawa, nionekera kufikira kumadzulo; kotero kudzakhalanso kufika kwace kwa Mwana wa munthu.

28 Kumene kuli konse uli mtembo, miimba Idzasonkhanira konko.

29 Koma pomwepo, atapita masauko a masiku awo, dzuwa lidzadetsedwa, ndi mwezi sudzaonetsa kuwala kwace, ndi nyenyezi zidzagwa kucokera kumwamba, ndi mphamvu za kumwamba zidzagwedezeka:

30 ndipo pomwepo padzaoneka m'thambo cizindikiro ca Mwana wa munthu; ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzadziguguda pacifuwa, nidzapenya Mwana wa munthu alinkudza pa mitambo ya kumwamba, ndi mphamvu ndi ulemerero waukuru.

31 Ndipo Iye adzatumiza angelo ace ndi kulira kwakukuru kwa lipenga, ndipo iwo adzasonkhanitsa osankhidwa ace ku mphepo zinai, kuyambira malekezero a thambo kufikira malekezero ace ena.

32 Koma phunzirani ndi mkuyu fanizo lace; pamene tsopano nthambi yace iri yanthete, nipuka masa-i mba ace, muzindikira kuti dzinja liyandikira;

33 comweconso inu, pamene mudzaona zimenezo, zindikirani kuti Iye ali pafupi, inde pakhomo.

34 Indetu ndinena kwa inu, mbadwo uwu sudzatha kucoka, kufikira zinthu zonsezi zidzacitidwa.

35 Thambo ndi dziko lapansi zidzacoka, koma mau anga sadzacoka ai.

36 Koma za tsiku ilo ndi nthawi yace sadziwa munthu ali yense, angakhale angelo a Kumwamba, kapena Mwana, koma Atate yekha.

37 Ndipo 1 monga masiku a Nowa, kotero kudzakhala kufika kwace kwa Mwana wa munthu.

38 Pakuti monga m'masiku aja, cisanafike cigumula, anthu analinkudya ndi kumwa, analikukwatira ndi kukwatiwa, kufikira tsiku limene Nowa analowa m'cingalawa,

39 ndipo iwo sanadziwa kanthu, kufikira kumene cigumula cinadza, cinapululutsa iwo onse, kotero kudzakhala kufika kwace kwa Mwana wa munthu.

40 Pomwepo 2 adzakhala awiri m'munda; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa:

41 awiri adzakhala opera pamphero; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa.

42 3 Cifukwa cace dikirani, pakuti simudziwa tsiku lace lakufika Ambuye wanu.

43 Koma 4 dziwani ici, kuti mwini nyumba akadadziwa nthawi yiti mbala ikudza, iye akadadikira, ndipo sakadalola kuti nyumba yace ibooledwe.

44 Cifukwa cace 5 khalani inunso okonzekeratu; cifukwa munthawi m'mene simuganizira, Mwana wa munthu adzadza.

45 6 Ndani kodi ali kapolo wokhulupirika ndi wanzeru, amene mbuye wace anamkhazika woyang'anira banja lace, kuwapatsa zakudya pa nthawi yace?

46 Wodala kapolo amene mbuye wace, pakufika, adzampeza iye alikucita cotero.

47 Indetu, ndinena kwa inu, kuti 7 adzamkhazika iye woyang'anira zinthu zace zonse.

48 Koma kapolo woipa akanena mumtima mwace, Mbuye wanga wacedwa;

49 nadzayamba kupanda akapolo anzace, nadya ndi kumwa pamodzi ndi oledzera;

50 mbuye wa kapoloyo adzafika tsiku losamuyembekeza iye, ndi nthawi yosadziwa iye,

51 nadzamdula, nadzaika pokhala pace ndi anthu onyenga; 8 pomwepo padzakhala kulira ndi kukukuta mano.

25

1 Pomwepo Ufumu wa Kumwamba udzafanizidwa ndi anamwali khumi, amene anatenga nyali zao, naturuka kukakomana ndi mkwati.

2 Ndipo asanu a iwo anali opusa, ndi asanu anali ocenjera.

3 Pakuti opusawo, m'mene anatenga nyali zao, sanadzitengeranso mafuta;

4 koma anzeruwo anatenga mafuta m'nsupa zao, pamodzi ndi nyali zao.

5 Ndipo pamene mkwati anacedwa, onsewo anaodzera, nagona tulo.

6 Koma pakati pa usiku panali kupfuula, Onani, mkwati! turukani kukakomana naye.

7 Pomwepo anauka anamwali onse amenewo, nakonza nyali zao.

8 Ndipo opusa anati kwa ocenjera, Tipatseniko ena a mafuta anu; cifukwa nyali zathu zirikuzima.

9 Koma ocenjera anayankha nati, Kapena sangakwanire ife ndi inu; koma makamaka mukani kwa ogulitsa malonda, mukadzigulire inu nokha.

10 Ndipo pamene iwo analikumuka kukagula, mkwati anafika; ndipo okonzekawo, analowa naye pamodzi muukwati; ndipo anatseka pakhomo.

11 Koma pambuyo pace anadzanso anamwali enawo, nati, Mbuye, Mbuye, mutitsegulire ife.

12 Koma iye anayankha nati, Indetu ndinena kwa inu, sindikudziwani.

13 Cifukwa cace dikirani, pakuti simudziwa tsiku lace, kapena nthawi yace.

14 Pakuti monga munthu, wakunka ulendo, aitana akapolo ace, napereka kwa iwo cuma cace.

15 Ndipo mmodzi anampatsa ndalama za matalente zisanu, ndi wina ziwiri, ndi wina imodzi; kwa iwo onse monga nzeru zao; namuka iye.

16 Pomwepo uyo amene analandira ndalama zisanu, anapita kugula nazo malonda, napindulapo ndalama zina zisanu.

17 Cimodzimodzinso uyo wa ziwirizo, anapindulapo zina ziwiri.

18 Koma uyo amene analandira imodziyo anamuka, nakumba pansi, naibisa ndalama ya mbuye wace.

19 Ndipo Itapita nthawi yaikuru, anabwera mbuye wa akapolo awo, nawerengera nao pamodzi.

20 Ndipo uyo amene adalandira ndalama za matalente zisanu anadza, ali nazo ndalama zina zisanu, nanena, Mbuye, munandipatsa ndalama za matalente, zisanu, onani ndapindulapo ndalama zisanu zina.

21 Mbuye wace anati kwa iye, Cabwino, kapolo iwe wabwino ndi wokhulupirika; unali wokhulupirika pa zinthu zazing'ono, ndidzakhazika iwe pa zinthu zambiri; Iowa iwe m'cikondwero ca mbuye wako.

22 Ndipo wa ndalama ziwiriyo anadzanso, nati, Mbuye, munandipatsa ine ndalama ziwiri; onani, ndapindulapo ndalama zina ziwiri.

23 Mbuye wace anati kwa iye, Cabwino, kapolo iwe wabwino ndi wokhulupirika; unali wokhulupirika pa zinthu zazing'ono, ndidzakhazika iwe pa zinthu zambiri; Iowa iwe m'cikondwero ca mbuye wako.

24 Ndipo uyonso amene analandira ndalama imodzi, anadza, nati, Mbuye, ndinakudziwani inu kuti ndinu munthu wouma mtima, wakututa kumene simunafesa, ndi wakusonkhanitsa kumene simunawaza;

25 ndinaopa ine, ndinapita, ndinabisa pansi ndalama yanu: onani, siyi yanu.

26 Koma mbuye wace anayankha, nati kwa iye, Kapolo iwe woipa ndi waulesi, unadziwa kuti ndimatuta kumene sindinafesa, ndi kusonkhanitsa kumene sindinawaza;

27 cifukwa cace ukadapereka ndalama zanga kwa okongola ndalama, ndipo ine pobwera ndikadatenga zanga ndi phindu lace.

28 Cifukwa cace cotsani kwa iye ndalamayo, muipatse kwa amene ali nazo ndalama khumi.

29 Pakuti kwa yense amene ali nazo, kudzapatsidwa, ndipo iye adzakhala nazo zocuruka: koma kwa iye amene alibe, kudzacotsedwa, cingakhale cimene anali naco.

30 Ndipo ponyani kapoloyo wopanda pace ku mdima wakunja; kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.

31 Koma pamene Mwana wa munthu adzadza mu ulemerero wace, ndi angelo onse pamodzi naye, pomwepo Iye adzakhala pa cimpando ca kuwala kwace:

32 ndipo adzasonkhanidwa pamaso pace anthu a mitundu yonse; ndipo Iye adzalekanitsa iwo wina ndi mnzace, monga mbusa alekanitsa nkhosa ndi mbuzi;

33 nadzakhalitsa nkhosa ku dzanja lace lamanja, koma mbuzi kulamanzere.

34 Pomwepo Mfumuyo idzanena kwa iwo a ku dzanja lace lamanja, Idzani kuno inu odalitsika a Atate wanga, lowani mu Ufumu wokonzedwera kwa inu pa cikhazikiro cace ca dziko lapansi:

35 pakuti ndinali ndi njala, ndipo munandipatsa Ine kudya; ndinali ndi ludzu, ndipo munandimwetsa Ine; ndinali mlendo, ndipo munacereza Ine;

36 wamarisece Ine, ndipo munandibveka; ndinadwala, ndipo munadza kuceza ndi Ine; ndinali m'nyumba yandende, ndipo munadza kwa Ine.

37 Pomwepo olungama adzamyankha Iye kuti, Ambuye, tinakuonani Inu liti wanjala, ndi kukudyetsani? kapena waludzu, ndi kukumwetsani?

38 Ndipo tinaona Inu liti mlendo, ndi kukucerezani? kapena wamarisece, ndi kukubvekani?

39 Ndipo tinakuonani Inu liti wodwala, kapena m'nyumba yandende, ndipo tinadza kwa Inu?

40 Ndipo Mfumuyo idzayankha nidzati kwa iwo, Indetu ndinena kwa inu, Cifukwa munacitira ici mmodzi wa abale anga, ngakhale ang'onong'ono awa, munandicitira ici Ine.

41 Pomwepo Iye adzanena kwa iwo a ku dzanja lamanzere, Cokani kwa Ine otembereredwa inu, ku mota wa nthawi zonse wokolezedwera mdierekezi ndi amithenga ace:

42 pakuti ndinali ndi njala, ndipo simunandipatsa Ine kudya: ndinali ndi ludzu, ndipo simunandimwetsa Ine:

43 ndinali mlendo, ndipo simunandilandira Ine; wamarisece ndipo simunandibveka Ine; wodwala, ndi m'nyumba yandende, ndipo simunadza kundiona Ine.

44 Pomwepo iwonso adzayankha kuti, Ambuye, tinakuonani liti wanjala, kapena waludzu, kapena mlendo, kapena wamarisece, kapena m'nyumba yandende, ndipo ife sitinakutumikirani Inu?

45 Pomwepo Iye adzayankha iwo kuti, Indetu ndinena kwa inu, Cifukwa munalibe kucitira ici mmodzi wa awa ang'onong'ono, munalibe kundicitira ici Ine.

46 Ndipo amenewa adzacoka kumka ku cilango ca nthawi zonse; koma olungama ku moyo wa nthawi zonse.

26

1 Ndipo panali pamene Yesu anatha mau onse amenewa, anati kwa ophunzira ace,

2 Mudziwa kuti akapita masiku awiri, Paskha ufika, ndipo Mwana wa munthu adzaperekedwa kupacikidwa pamtanda.

3 Pomwepo anasonkhana ansembe akuru, ndi akuru a anthu, ku bwalo la mkuru wa ansembe, dzina lace Kayafa;

4 nakhala upo wakuti amgwire Yesu ndi cinyengo, namuphe.

5 Koma ananena iwo, Pa dzuwa la cakudya iai, kuti pasakhale phokoso la anthu.

6 Ndipo pamene Yesu anali m'Betaniya, m'nyumba ya Simoni wakhate,

7 anadza kwa Iye mkazi, anali nayo nsupa yaalabastero ndi mafuta onunkhira bwino a mtengo wapatari, nawatsanulira pamutu pace, m'mene Iye analikukhala pacakudya.

8 Koma m'mene ophunzira anaona, anada mtima, nanena, Cifukwa ninji kuononga kumeneku?

9 Pakuti mafuta awa akadagulitsa ndalama zambiri, ndi kuzipatsa anthu aumphawi.

10 Koma Yesu podziwa, anati kwa iwo, Mumbvutiranji mkaziyu? popeza andicitira Ine nchito yabwino.

11 Pakuti nthawi zonse muli nao aumphawi pamodzi nanu; koma simuli ndi Ine nthawi zonse.

12 Pakuti mkaziyo, m'mene anathira mafuta awa pathupi panga, wandicitiratu ici pa kuikidwa kwanga.

13 Indetu ndinena kwa inu, kumene kuli konse uthenga uwu wabwino udzalalikidwa m'dziko lonse lapansi, ici cimene mkaziyo anacitaci cidzakambidwanso cikumbukiro cace.

14 Pomwepo mmodzi wa khumi ndi awiriwo, dzina lace Yudase Isikariote, anamuka kwa ansembe akuru,

15 nati, Mufuna kundipatsa ciani, ndipo ine ndidzampereka Iye kwa inu? Ndipo iwo anamwerengera iye ndalama zasiliva makumi atatu.

16 Ndipo kuyambira pamenepo iye anafunafuna nthawi yabwino yakuti ampereke Iye.

17 Ndipo tsiku loyamba la mkate wopanda cotupitsa, ophunzira anadza kwa Yesu, nati, Mufuna tikakonzere kuti Paskha, kuti mukadye?

18 Nati Iye, Mukani kumzinda kwa munthu wangana, mukati kwa iye, Mphunzitsi anena. Nthawi yanga yayandikirai ndidzadya Paskha kwanu pamodzi ndi ophunzira anga.

19 Ndipo ophunzira anacita monga Yesu anawauza, nakonza Paskha.

20 Ndipo pakufika madzulo, Iye analikukhala pacakudya pamodzi ndi ophunzira khumi ndi awiri;

21 ndipo m'mene analinkudya, Iye anati, Indetu ndinena kwa inu, mmodzi wa inu adzandipereka Ine.

22 Ndipo iwo anagwidwa ndi cisoni cacikuru, nayamba kunena kwa Iye mmodzi mmodzi, Kodi ndine, Ambuye?

23 Ndipo Iye anayankha nati, Iye amene asunsa pamodzi ndi Ine dzanja lace m'mbale, yemweyu adzandipereka Ine.

24 Mwana wa munthu acokatu, monga kunalembedwa za Iye; koma tsoka ali nalo munthu amene Mwana wa munthu aperekedwa ndi iye! kukadakhala bwino kwa munthuyo ngati sakadabadwa.

25 Ndipo Yudase, womperekayo anayankha nati, Kedi ndine, Rabi? Iye ananena kwa iye, Iwe watero.

26 Ndipo pamene iwo analinkudya, Yesu anatenga mkate, nadalitsa, naunyema; ndipo m'mene anapatsa kwa ophunzira, anati, Tengani, idyani; ici ndi thupi langa.

27 Ndipo pamene anatenga cikho, anayamika, napatsa iwo, nanena, Mumwere ici inu nonse,

28 pakuti ici ndici mwazi wanga wa pangano, wothiridwa cifukwa ca anthu ambiri ku kucotsa macimo.

29 Ndipo ndinena kwa inu, sindidzamwanso cipatso ici campesa, kufikira tsiku limene ndidzamwa catsopano, pamodzi ndi inu, mu Ufumu wa Atate wanga.

30 Ndipo pamene anayimba nyimbo, anaturuka kunka ku phiri la Azitona.

31 Pamenepo Yesu ananena kwa iwo, Inu nonse mudzakhumudwa cifukwa ca Ine usiku uno; pakuti kwalembedwa, Ndidzakantha mbusa, Ndipo zidzabalalika Nkhosa za gulu.

32 Koma nditauka ndidzatsogolera inu ku Galileya.

33 Koma Petro ananena kwa Iye, Ngakhale onse adzakhumudwa cifukwa ca Inu, ine sindidzakhumudwa nthawi zonse.

34 Yesu anati kwa iye, Indetu ndinena kwa iwe, kuti usiku uno, tambala asanalire, udzandikana Ine katatu.

35 Petro ananena kwa Iye, Ngakhale ine ndikafa ndi Inu, sindidzakukanani Inu iai. Anateronso ophunzira onse.

36 Pomwepo Yesu anadza ndi iwo ku malo ochedwa Getsemane, nanena kwa ophunzira ace, Bakhalani inu pompano, ndipite uko ndikapemphere.

37 Ndipo anatenga Petro ndi ana awiria Zebedayo pamodzi naye, nayamba kugwidwa ndi cisoni ndi kuthedwa nzeru.

38 Pamenepo ananena kwa iwo, Moyo wanga uti wozingidwa ndi cisoni ca kufika naco kuimfa; khalani pano mucezere pamodzi ndi Ine.

39 Ndipo anamuka patsogolo pang'ono, nagwa nkhope yace pansi, napemphera, nati, Atate, ngati nkutheka, cikho ici cindipitirire Ine; koma si monga ndifuna Ine, koma lou.

40 Ndipo anadza kwa ophunzira, nawapeza iwo ali m'tulo, nanena kwa Petro, Nkutero kodi? simukhoza kucezera ndi Ine mphindi imodzi?

41 Cezerani ndi kupemphera, kuti mungalowe m'kuyesedwa: mzimutu uti wakufuna, koma thupi liri lolefuka.

42 Anamukanso kaciwiri, napemphera, nati, Atate wanga, ngati ici sicingandipitirire, koma ndimwere ici, kufuna kwanu kucitidwe.

43 Ndipo anabweranso, nawapeza iwo ali m'tulo, pakuti zikope zao zinalemera ndi tulo.

44 Ndipo anawasiyanso, napemphera kacitatu, nateronso mau omwewo.

45 Pomwepo anadza kwa ophunzira, nanena kwa iwo, Gonani nthawi yatsalayi, mupumule; onani, nthawi yafika, ndipo Mwana wa munthu aperekedwa m'manja ocimwa.

46 Ukani, timuke; taonani, iye wakundipereka wayandikira.

47 Ndipo Iye ali cilankhulire, onani, Yudase, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anadza, ndi pamodzi ndi iye khamu lalikuru la anthu, ndi malupanga ndi mikunkhu, kucokera kwa ansembe akuru ndi akuru a anthu.

48 Koma wompereka Iye anawapatsa cizindikiro, nanena, Iye amene ndidzampsompsona ndiyeyo, mumgwire Iye.

49 Ndipo pomwepo anadza kwa Yesu, nati, Tikuoneni, Rabi; nampsompsonetsa.

50 Ndipo Yesu anati kwa iye, Mnzanga, wafikiranji: iwe? Pomwepo iwo anadza, namthira Yesu manja, namgwira Iye.

51 Ndipo onani, mmodzi wa iwo anali pamodzi ndi Yesu, anatansa dzanja lace, nasolola Iupanga lace, nakantha kapolo wa mkuru wa ansembe, nadula khutu lace.

52 Pomwepo Yesu ananena kwa iye, Tabweza Iupanga lako m'cimakemo, pakuti onse akugwira lupanga adzaonongeka ndi Iupanga,

53 Kapena uganiza kuti sindingathe kupemphera Atate wanga, ndipo Iye adzanditumizira tsopano lino mabungwe a angelo oposa khumi ndi awiri?

54 Koma pakutero malembo adzakwaniridwa bwanji, pakuti kuyenera comweco?

55 Nthawi yomweyo Yesu anati kwa makamuwo a anthu, Kodi munaturukira kundigwira Ine ndi malupanga ndi mikunkhu, ngati wacifwamba? Tsiku ndi tsiku ndimakhala m'Kacisi kuphunzitsa, ndipo simunandigwira.

56 Koma izi zonse zinacitidwa, kuti 1 zolembedwa za aneneri zikwaniridwe. Pomwepo ophunzira onse anamsiya Iye, nathawa.

57 Ndipo iwo akugwira Yesu anaaka naye kwa Kayafa, mkuru wa ansembe, kumene adasonkhana alembi ndi akuru omwe.

58 Koma Petro anamtsata kutari, kufikira ku bwalo la mkuru wa ansembe, nalowamo, nakhala pansi ndi anyamata, kuti aone cimariziro.

59 Ndipo ansembe akuru ndi akuru mirandu onse mafunafuna umboni wonama wakutsutsa Yesu, kuti amuphe Iye;

60 koma sanaupeza zingakhale 2 mboni zonama zambiri zinadza. Koma pambuyo pace anadza awiri,

61 nati, Uyu ananena kuti, 3 Ndikhoza kupasula Kacisi, ndi kummanganso masiku atatu.

62 Ndipo mkuru wa ansembe anaimirira, nati kwa Iye, Subvomera kanthu kodi? nciani ici cimene awa akunenera Iwe?

63 Koma 4 Yesu anangokhala cete. Ndipo mkuru wa ansembe ananena kwa Iye, Ndikulumbiritsa Iwe pa Mulungu wamoyo, kuti utiuze ife ngati Iwe ndiwe Kristu, Mwana wa Mulungu.

64 Yesu anati kwa iye, Mwatero, koma ndinenanso kwa inu, 5 Kuyambira tsopano mudzaona Mwana wa munthu ali kukhala ku dzanja lamanja la mphamvu, ndi kufika pa mitambo ya kumwamba.

65 Pomwepo mkuru wa ansembe 6 anang'amba zobvala zace, nati, Acitira Mulungu mwano; tifuniranji mboni zina? onani, tsopano mwamva mwanowo;

66 muganiza bwanji? lwo anayankha nati, 7 Ali woyenera kumupha,

67 8 Pomwepo iwo anathira malobvu pankhope pace, nambwanyula Iye; ndipo ena anampanda kofu,

68 nati, 9 Utilote ife, Kristu Iwe; wakumenya Iwe ndani?

69 Ndipo 10 Petro adakhala pabwato: ndipo mdzakazi anadza kwa iye, nanena, Iwenso unali ndi Yesu wa ku Galileya.

70 Koma iye anakana pamaso pa anthu onse, kuti, Cimene unena sindicidziwa.

71 Ndipo pamene iye anaturuka kunka kucipata, mkazi wina anamuona, nati kwa iwo a pomwepo, Uyonso anali ndi Yesu Mnazarayo.

72 Ndipo anakananso ndi cilumbiro, kuti, Sindidziwa munthuyo.

73 Ndipo popita nthawi yaing'ono, iwo akuimapo anadza, nati kwa Petro, Zoonadi, iwenso uli wa iwo; pakuti malankhulidwe ako akuzindikiritsa iwe.

74 11 Pamenepo iye anayamba kutemberera ndi kulumbira, kuti, Sindidziwa munthuyo. Ndipo pompo tambala analira.

75 Ndipo Petro anakumbukira mau amene Yesu adati, 12 Asanalire tambala udzandikana katatu. Ndipo anaturukira kunja, nalira ndi kuwawa mtima.

27

1 Ndipo pakudza mamawa, ansembe akuru ndi akuru a anthu onse anakhala upo wakumcitira Yesu, kuti amuphe;

2 ndipo anammanga Iye, namuka naye, nampereka Iye kwa Pilato kazembeyo.

3 Pamenepo Yudase yemwe anampereka Iye, poona kuti Iye anatsutsidwa kuti afe, analapa, nabweza ndalama zija zasiliva makumi atatu kwa ansembe akuru ndi akuru,

4 nanena, Ndinacita koipa ine, pakupereka mwazi wosalakwa. Koma iwo anati, Tiri naco ciani ife? udzionere wekha.

5 Ndipo iye anataya pansi ndalamazo paKacisi, nacokapo, nadzipacika yekha pakhosi.

6 Ndipo ansembe akuru anatenga ndalamazo, nati, Sikuloledwa kuziika m'cosonkhera ndalama za Mulungu, cifukwa ndizo mtengo wa mwazi.

7 Koma anapangana, nazigula munda wa woumba mbiya, ukhale manda a alendo.

8 Cifukwa cace munda umenewu anaucha, Munda-wa-mwazi, kufikira lero lino.

9 Pamenepo cinakwaniridwa conenedwa ndi Yeremiya mneneri, ndi kuti, Ndipo iwo anatenga ndalamazo zasiliva makumi atatu, Mtengo wa uja wowerengedwa mtengo wace, Amene iwo a ana a Israyeli anawerenga mtengo wace;

10 Ndipo anazipereka kugula munda wa woumba mbiya, Monga anandilamulira ine Ambuye.

11 Ndipo Yesu anaimirira pamaso pa kazembe, ndipo kazembeyo anamfunsa Iye kuti, Kodi Iwe ndiwe mfumu ya Ayuda? Ndipo Yesu anati kwa iye, Mwatero.

12 Ndipo pakumnenera Iye ansembe akuru ndi akuru, Iye sanayankha kanthu.

13 Pomwepo Pilato ananena kwa Iye, Sukumva kodi zinthu zambiri zotere akunenera Iwe?

14 Ndipo sanayankha Iye, ngakhale mau amodzi, kotero kuti kazembe anazizwa ndithu.

15 Ndipo pa Paskha kazembe adazolowera kumasulira anthu mmodzi wandende, amene iwo anafuna.

16 Ndipo pa nthawi yomweyo anali ndi wandende wodziwika, dzina lace Baraba.

17 Cifukwa cace pamene anasonkhana, Pilato ananena kwa iwo, Mufuna kuti ndikumasulireni yani? Baraba kodi, kapena Yesu, wochedwa Kristu?

18 Pakuti anadziwa kuti anampereka Iye mwanjiru.

19 Ndipo pamene Pilato analikukhala pa mpando wakuweruza, mkazi wace anatumiza mau kwa iye, kunena, Musacite kanthu ndi munthu wolungamayo; pakuti lero m'kulota ine ndasauka kwambiri cifukwa ca Iye.

20 Koma ansembe akuru anapangira anthu kuti apemphe Baraba, koma kuti aononge Yesu.

21 Koma kazembe anati kwa iwo, Mufuna kuti ndikumasulireni uti wa awa awiri? Ndipo iwo anati, Baraba.

22 Pilato ananena kwa iwo, Nanga ndidzacita ciani ndi Yesu, wochedwa Kristu?

23 Onse anati, Apacikidwe pamtanda. Ndipo iye anati, Cifukwa ninji? anacita coipa cotani? Koma iwo anapfuulitsa kopambana, Apacikidwe pamtanda.

24 Koma Pilato poona kuti sanafitse, koma kuti linapambana phokoso, anatenga madzi, nasamba manja pamaso pa khamulo, nati, Ine ndiribe kucimwira mwazi wa munthu uyu wolungama, mudzionere nokha.

25 Ndipo anthu onse anabvomereza, ndi kuti, Mwazi wace uli pa ife ndi pa ana athu.

26 Pomwepo iye anamasulira iwo Baraba, koma anakwapula Yesu, nampereka Iye kuti akampacike pamtanda.

27 Pomwepo asilikari a kazembe anamuka naye Yesu ku bwalo la mirandu, nasonkhanitsa kwa iye khamu lao lonse.

28 Ndipo anabvula malaya ace, nambveka malaya ofiira acifumu.

29 Ndipo analuka korona waminga, nambveka pamutu pace, namgwiritsa bango m'dzanja lamanja lace; ndipo anagwada pansi pamaso pace, namcitira cipongwe, nati, Tikuoneni, Mfumu ya Ayuda!

30 Namthira malobvu, natenga bango, nampanda Iye pamutu.

31 Ndipo pamene anatha kumcitira Iye cipongwe, anabvula malaya aja, nambveka Iye malaya ace, namtsogoza Iye kukampacika pamtanda.

32 Ndipo pakuturukapao anapeza munthu wa ku Kurene, dzina lace Simoni, namkangamiza iye kuti anyamule mtanda wace.

33 Ndipo pamene anadza kumalo dzina lace Golgota, ndiko kunena kuti, Malo-abade,

34 anamwetsa Iye vinyo wosanganiza ndi ndulu; ndipo Iye, m'mene analawa, sanafuna kumwa.

35 Ndipo pamene anampacika Iye, anagawana zobvala zace ndi kulota maere:

36 nakhala iwo pansi, namdikira kumeneko.

37 Ndipo anaika pamwamba pamutu pace liwongo lace lolembedwa: UYU NDI YESU MFUMU YA AYUDA.

38 Pamenepo anapacika pamodzi ndi Iyeacifwamba awiri, mmodzi ku dzanja lamanja, ndi wina kulamanzere.

39 Ndipo anthu akupitirirapo 1 anamcitira mwano Iye ndi kupukusa mitu yao,

40 nati, Nanga 2 Iwe, wopasula Kacisi, ndi kummanganso masiku atatu, tadzipulumutsa wekha; 3 ngati uli Mwana wa Mulungu, tatsika pamtandapo.

41 Comweconso ansembe akuru, pamodzi ndi alembi ndi akuru anamcitira cipongwe, nati,

42 Anapulumutsa ena, sangathe kudzipulumutsa yekha. Ndiye Mfumu ya Ayuda; atsike tsopano pamtandapo, ndipo tidzamkhulupirira Iye.

43 4 Amakhulupirira Mulungu; Iye ampulumutse tsopano, ngati amfuna; pakuti anati, Ine ndine Mwana wa Mulungu.

44 Ndiponso 5 acifwambawo opacikidwa pamodzi ndi Iye, anamlalatira Iye mau amodzimodzi.

45 Ndipo 6 ora lacisanu ndi cimodzi panali mdima pa dziko lonse, kufikira ora lacisanu ndi cinai.

46 Ndipo poyandikira ora lacisanu ndi cinai, Yesu 7 anapfuula ndi mau akuru, kunena, Eli, Eli, lama sabakitani? ndiko kunena kuti, Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji Ine?

47 Ndipo ena a iwo akuimirira komweko, pamene anamva, ananena, Uyo aitana Eliya.

48 Ndipo pomwepa mmodzi wa iwo anathamanga, 8 natenga cinkhupule, nacidzaza ndi vinyo wosasa, naciika pabango, namwetsa Iye.

49 Koma ena anati, Taleka, tione ngati Eliya adzafika kudzampulumutsa.

50 Ndipo Yesu, 9 pamene anapfuula ndi mau akuru, anapereka mzimu wace.

51 Ndipo onani, 10 cinsaru cocinga ca m'Kacisi cinang'ambika pakati, kucokera kumwamba kufikira pansi; ndipo dziko linagwedezeka, ndi miyala inang'ambika;

52 ndi Manda anatseguka, ndi mitembo yambiri ya anthu oyera mtima, akugona kale, inauka;

53 ndipo anaturuka m'manda mwao pambuyo pa kuuka kwace, nalowa m'mzinda woyera, naonekera kwa anthu ambiri.

54 Ndipo pamene mkuru wa asilikari, ndi iwo anali naye 11 akudikira Yesu, anaona cibvomezi, ndi zinthu zimene zinacitidwa, anaopa kwambiri, nanena, Indedi Uyo ndiye Mwana wa Mulungu.

55 Ndipo anali pomwepo akazi ambiri, akuyang'anira patari, 12 Omwe anatsata Yesu kucokera ku Galileya, namatumikira Iye;

56 mwa iwo 13 amene munali Mariya wa Magadala, ndi Mariya amace wa Yakobo, ndi wa Yose, ndi amace wa ana a Zebedayo.

57 Ndipo pamene panali madzulo, anadza munthu wacuma wa ku Arimateya, dzina lace Yosefe, amene analinso wophunzira wa Yesu;

58 yemweyo anapita kwa Pilato, napempha mtembo wa Yesu. Pomwepo Pilato analamula kuti uperekedwe.

59 Ndipo Yosefe anatenga mtembo, naukulunga m'nsaru yabafuta yoyeretsa,

60 14 nauika m'manda ace atsopano, osemedwa m'mwala, nakunkhunizira mwala waukuru pakhomo pa manda, nacokapo,

61 Ndipo Mariya wa Magadala anali pamenepo, ndi Mariya winayo, anakhala pansi popenyana ndi mandawoo

62 Ndipo m'mawa mwace, ndilo dzuwa lotsatana ndi tsiku lokonzera, ansembe akuru ndi Afarisi anasonkhanira kwa Pilato,

63 nanena, Mfumu, takumbukira ife kuti wonyenga uja anati, pamene anali ndi moyo, 15 Ndidzaukapofikamasikuatatu.

64 Cifukwa cace mulamule kuti asindikize pamandapo, kufikira tsiku lacitatulo, kuti kapena ophunzira ace angadze, nadzamuba Iye, nadzanena kwa anthu, kuti Iye anauka kwa akufa: ndipo cinyengo comariza cidzaposa coyambaco.

65 Pilato anati kwa iwo, Tengani alonda; mukani, kasungeni monga mudziwa.

66 Ndipo iwo anamuka, nasunga manda, 16 nasindikizapo cizindikiro pamwalapo, iwo pamodzi ndi alondawo.

28

1 Ndipo popita dzuwa la Sabata, mbanda kuca, tsiku lakuyamba la sabata, anadza Mariya wa Magadala, ndi Mariya winayo, kudzaona manda.

2 Ndipo onani, panali cibvomezi cacikuru; pakuti mngelo wa Ambuye anatsika Kumwamba, nafika kukunkhuniza mwalawo, nakhala pamwamba pace.

3 Kuonekera kwace kunali ngati mphezi, ndi cobvala cace coyeretsa ngati matalala;

4 ndipo ndi kuopsa kwace alondawo ananthunthumira, nakhala ngati anthu akufa.

5 Koma mngelo anayankha, nati kwa akaziwo, Musaope inu; pakuti ndidziwa inu mulikufuna Yesu, amene anapacikidwa.

6 Iye mulibe muno iai; pakuti anauka, monga ananena. Idzani muno mudzaone malo m'mene anagonamo Ambuye.

7 Ndipo pitani msanga, muuze ophunzira ace, kuti, Wauka kwa akufa; ndipo onani, akutsogolerani ku Galileya; mudzamuona Iye komweko; onani, ndakuuzani inu.

8 Ndipo iwo anacoka msanga kumanda, ndi mantha ndi kukondwera kwakukuru, nathamanga kukauza ophunzira ace.

9 Ndipo onani, Yesu anakomana nao, nanena, Tikuoneni. Ndipo iwo anadza, namgwira Iye mapazi ace, namgwadira.

10 Pomwepo Yesu ananena kwa iwo, Musaope; pitani, kauzeni abale anga kuti amuke ku Galileya, ndipo adzandiona Ine kumeneko.

11 Ndipo pameneiwo analikupita, onani, ena a alonda anafika kumzinda, nauza ansembe akuru zonse zimene zinacitidwa.

12 Ndipo pamene anasonkhana pamodzi ndi akuru, anakhala upo, napatsa asilikariwo ndalama zambiri,

13 nati, Kazinenani, kuti ophunzira ace anadza usiku, namuba Uja m'mene ife tinali m'tulo.

14 Ndipo ngati ici cidzamveka kwa kazembe, ife tidzamgwetsa mtima, ndipo tidzakukhalitsani opanda nkhawa.

15 Ndipo iwo analandira ndalamazo, nacita monga anawalangiza: ndipo mbiri iyo inabuka mwa Ayuda, kufikira lero lomwe.

16 Koma ophunzira khumi ndi mmodziwo anamuka ku Galileya, kuphiri kumene Yesu anawapangifa.

17 Ndipo pamene anamuona Iye, anamlambira; koma ena anakayika.

18 Ndipo Yesu anadza nalankhula nao, nanena, Mphamvu zonse zapatsidwa kwa Ine Kumwamba ndi pa dziko lapansi.

19 Cifukwa cace mukani, phunzitsani anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza iwo m'dzina la Atate, ndi la Mwana, ndi la Mzimu Woyera:

20 ndi kuwaphunzitsa, asunge zinthu zonse zimene ndinakulamulirani inu; ndipo onani, Ine ndiri pamodzi ndi inu masiku onse, kufikira cimariziro ca nthawi ya pansi pano.