1

1 PANALI munthu m'dziko la Uzi, dzina lace ndiye Yobu; ndipo munthuyu anali wangwiro ndi woongoka, wakuopa Mulungu ndi kupewa zoipa.

2 Ndipo anabala ana amuna asanu ndi awiri, ndi ana akazi atatu.

3 Zoweta zacenso zinali nkhosa zikwi zisanu ndi ziwiri, ndi ngamila zikwi zitatu, ndi ng'ombe zamagoli mazana asanu, ndi aburu akazi mazana asanu, anchito ace omwe ndi ambiri; cotero munthuyu anaposa anthu onse'a kum'mawa.

4 Ndipo ana ace amuna anamuka kukacita madyerero m'nyumba ya yense pa tsiku lace; natumiza mthenga kuitana alongo ao atatu adzadye nadzamwe nao.

5 Ndipo kunatero, atatha masiku a madyererowa Yobu anatumiza mau, nawapatula, nauka mamawa, nafukiza nsembe zopsereza, monga mwa kuwerenga kwa iwo onse; pakuti Yobu anati, Kapena anacimwa ana anga, nacitira Mulungu mwano m'mtima mwao. Anatero Yobu masiku onse.

6 Ndipo panali tsiku lakuti ana a Mulungu anadza kudzionetsa kwa Yehova, nadzanso Satana pakati pao.

7 Nati Yehova kwa Satana, Ufuma kuti? Nayankha Satana kwa Yehova, nati, Kupitapita m'dziko ndi kuyendayenda m'mwemo.

8 Ndipo Yehova anati kwa Satana, Kodi waonerera mtumiki wanga Yobu? pakuti palibe wina wonga iye m'dzikomo, munthu wangwiro ndi woongoka, wakuopa Mulungu ndi kupewa zoipa.

9 Nayankha Satana, nati kwa Yehova, Kodi Yobu aopa Mulungu pacabe?

10 Kodi simunamcinga iye ndi nyumba yace, ndi zace zonse, pomzinga ponse? nchito ya manja ace mwaidalitsa, ndi zoweta zace zacuruka m'dziko.

11 Koma mutambasule dzanja lanu ndi kumkhudzira zace zonse, ndipo adzakucitirani mwano pankhope panu.

12 Nati Yehova kwa Satana, Taona, zonse ali nazo zikhale m'dzanja mwako; pa iye pokha usatambasula dzanja lako. Naturuka Satana pamaso pa Yehova.

13 Tsono panali tsiku loti ana ace amuna ndi akazi analinkudya ndi kumwa vinyo m'nyumba ya mkuru wao;

14 nafika mthenga kwa Yobu, nati, Ng'ombe zinalikulima, ndi aburu akazi analikudya pambali pao;

15 koma anazigwera Aseba, nazitenga, nawapha anyamata ndi lupanga lakuthwa, ndipo ndapulumuka ine ndekha kudzakuuzani.

16 Akali cilankhulire uyu, anadza winanso, nati, Wagwa moto wa Mulungu wocokera kumwamba, wapsereza nkhosa ndi anyamata, nuzinyeketsa; ndipo ndapulumuka ine ndekha kudzakuuzani.

17 Akali cilankhulire uyu, anadza winanso, nati, Akasidi anadzigawa magulu atatu, nazigwera ngamila, nazitenga, nawapha anyamata ndi lupanga lakuthwa, ndipo ndapulumuka ine ndekha kudzakuuzani.

18 Akali cilankhulire, anadza winanso, nati, Ana anu amuna ndi akazi analinkudya ndi kumwa vinyo m'nyumba ya mkuru wao;

19 ndipo taonani, inadza mphepo yaikuru yocokera kucipululu, niomba pa ngondya zonse zinai za nyumbayo, nigwa pa anyamatawo, nafa; ndipo ndapulumuka ine ndekha kudzakuuzani.

20 Pamenepo Yobu ananyamuka, nang'amba maraya ace, nameta mutu wace, nagwa pansi, nalambira,

21 nati, Ndinaturuka m'mimba ya mai wanga wamarisece, wamarisece ndidzanrukanso; Yehova anapatsa, Yehova watenga, lidalitsike dzina la Yehova.

22 Mwa ici conse Yobu sanacimwa, kapena kunenera Mulungu colakwa.

2

1 Panalinso tsiku lakuti anadza ana a Mulungu kudzionetsa kwa Yehova, nadza Satana yemwe pakati pao kudzionetsa kwa Yehova.

2 Ndipo Yehova anati kwa Satana, Ufuma kuti? Nayankha Satana, nati kwa Yehova, Kupitapita m'dziko, ndi kuyendayenda m'mwemo.

3 Ndipo Yehova anati kwa Satana, Kodi waonerera mtumiki wanga Yobu? pakuti palibe wina wonga iye m'dzikomo, munthu wangwiro ndi woongoka, wakuopa Mulungu, ndi kupewa zoipa; naumirirabe kukhala wangwiro, cinkana undisonkhezera ndimuononge kopanda cifukwa.

4 Nayankha Satana, nati kwa Yehoya, Khungu kulipa khungu, inde munthu adzapereka zonse ali nazo kuombola moyo wace.

5 Koma tambasulani dzanja lanu, ndi kukhudza pfupa lace ndi mnofu wace, ndipo adzakucitirani mwano pamaso panu.

6 Ndipo Yehova anati kwa Satana. Taona, akhale m'dzanja lako; moyo wace wokha uuleke.

7 Naturuka Satana pamaso pa Yehova, nazunza Yobu ndi zironda zowawa, kuyambira ku phazi lace kufikira pakati pamutu pace.

8 Ndipo anadzitengera phale, kudzikanda nalo; nakhala pansi m'mapulusa.

9 Pamenepo mkazi wace ananena naye, Kodi uumiriranso kukhala wangwiro? citira Mulungu mwano, ufe.

10 Koma ananena naye, Ulankhula monga amalankhula akazi opusa. Ha! tidzalandira zokoma kwa Mulungu kodi, osalandiranso zoipa? pa ici conse Yobu sanacimwa ndi milomo yace.

11 Atamva tsono mabwenzi atatu a Yobu za coipa ici conse cidamgwera, anadza, yense kucokera kwao, Elifazi wa ku Temani, ndi Bilidadi Msuki, ndi Zofari wa ku Naama, napangana kudzafika kumlirira ndi kumsangalatsa.

12 Ndipo pokweza maso ao ali kutali, sanamdziwa, nakweza mau ao, nalira; nang'amba yense maraya ace, nawaza pfumbi kumwamba ligwe pamitu pao.

13 Nakhala pansi pamodzi naye panthaka masiku asanu ndi awiri usana ndi usiku, palibe mmodzi ananena naye kanthu, popeza anaona kuti kuwawaku nkwakukuru ndithu.

3

1 Atatero, Yobu anatsegula pakamwa pace, natemberera tsiku lace.

2 Nalankhula Yobu nati,

3 Litayike tsiku lobadwa ine, Ndi usikuwo udati, Waima naye mwana wamwamuna.

4 Tsiku lija likhale mdima; Mulungu asalifunse kumwamba, Ndi kuunika kusaliwalire.

5 Mdima ndi mthunzi wa imfa ziliyese lao lao; Mtambo ulikhalire; Zonse zodetsa usana bi ziliopse.

6 Usiku uja, mdima weni weni uugwere; Usakondwerere mwa masiku a m'caka; Usalowe m'ciwerengedwe ca miyezi.

7 Ha! usiku uja ukhale cumba; Kuyimbira kokondwera kusalowem'mwemo.

8 Autemberere iwo akutemberera usana, Odziwa kuutsa cinjokaco.

9 Nyenyezi za cizirezire zide; Uyembekezere kuunika, koma kuusowe; Usaone kuphenyuka kwa mbanda kuca;

10 Popeza sunatseka pa makomo ace mimba ya mai wanga. Kapena kundibisira mabvuto pamaso panga.

11 Ndinalekeranji kufera m'mimba? Ndi kupereka mzimu wanga pobadwa ine?

12 Anandilandiriranji maondo? Kapena mabere kuti ndiyamwe?

13 Pakuti ndikadagona pansi pomwepo ndi kukhala cete; Ndikanagona tulo; pamenepo ndikadaona popumula;

14 Pamodzi ndi mafumu ndi maphungu a padziko, Akudzimangira m'mabwinja;

15 Kapena pamodzi ndi akalonga eni ace a golidi, Odzaza nyumba zao ndi siliva;

16 Kapena ngati nsenye yobisika ndikadakhala kuli zi; Ngati makanda osaona kuunika.

17 Apo oipa aleka kumabvuta; Ndi apo ofoka mphamvu akhala m'kupumula.

18 Apo a m'kaidi apumula pamodzi, Osamva mau a wofulumiza wao.

19 Ang'ono ndi akulu ali komwe; Ndi kapolo amasuka kwa mbuyace.

20 Amninkhiranji kuunika wobvutika, Ndi moyo kwa iye wakuwawa mtima,

21 Wakuyembekezera imfa, koma kuli zi, Ndi kuikumba koposa cuma cobisika,

22 Wakusekerera ndi cimwemwe Ndi kukondwera pakupeza manda?

23 Amuonetseranji kuunika munthu wa njira yobisika, Amene wamtsekera Mulungu?

24 Pakuti ndikati ndidye, kumadza kuusa moyo kwanga; Ndi kudzuma kwanga kumathiridwa ngati madzi.

25 Pakuti cimene ndinaciopa candigwera, Ndi cimene ndacita naco mantha candidzera.

26 Wosakhazikika, ndi wosakhala cete, ndi wosapumula ine, Koma mabvuto anandidzera.

4

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha, nati,

2 Munthu akayesa kunena nawe mau, kodi udzamva nao cisoni? Koma akhoza ndani kudziletsa kunena?

3 Taona iwe walangiza aunyinji, Walimbitsa manja a ofoka.

4 Mau ako anacirikiza iye amene akadagwa, Walimbitsanso maondo otewa.

5 Koma tsopano cakufikira iwe, ndipo ukomoka; Cikukhudza, ndipo ubvutika.

6 Kodi kulimbika mtima kwako si ndiko kuti uopa Mulungu, Ndi ciyembekezo cako si ndiwo ungwiro wa njira zako?

7 Takumbukila tsopano, watayika ndani wosaparamula konse? Kapena oongoka mtima alikhidwa kuti?

8 Monga umo ndaonera, olimira mphulupulu, Nabzala bvuto, akololapo zomwezo.

9 Atayika ndi mpweya wa Mulungu, Nathedwa ndi mpumo wa mkwiyo wace.

10 Kubangula kwa mkango, ndi kulira kwa mkango waukali kwaletsedwa, Ndi mano a misona ya mkango atyoledwa.

11 Mkango wokalamba udzifera posowa mkoka, Ndi misona ya mkango waukazi imwazika.

12 Anditengera mau m'tseri, M'khutu mwanga ndinalandira kunong'oneza kwace.

13 M'malingaliro a masomphenya a usiku, Powagwira anthu tulo tatikuru,

14 Anandidzera mantha ndi kunjenjemera, Nanthunthumira nako mafupa anga onse.

15 Pamenepo panapita mzimu pamaso panga; Tsitsi la thupi langa lidati nyau nyau.

16 Unaima ciriri, koma sindinatha kuzindikira maonekedwe ace; Panali mzukwa pamaso panga; Kunali cete, ndipo ndidamva mau akuti,

17 Kodi munthu adzakhala wolungama ndi kuposa Mulungu? Kodi munthu adzakhala woyera woposa Mlengi wace?

18 Taona, sakhulupirira atumiki ace; Nawanenera amithenga ace zopusa;

19 Kopambana kotani nanga iwo akukhala m'nyumba zadothi, Amene kuzika kwao kuti m'pfumbi, Angothudzulidwa ngati gulugufe,

20 Kuyambira m'mawa kufikira madzulo athudzuka; Aonongeka kosatha, osasamalirako munthu.

21 Kukometsetsa kwao sikumacotsedwa nao? Amafa koma opanda nzeru.

5

1 Itana tsono; pali wina wakukuyankha kodi? Ndipo udzatembenukira kwa yani wa oyera mtimawo?

2 Pakuti mkwiyo umapha wopusa, Ndi nsanje imakantha wopanda pace.

3 Ndinapenya wopusa woyala mizu; Koma pomwepo ndinatemberera pokhala pace.

4 Ana ace akhala otekeseka, Napsinjika kucipata, Wopanda wina wakuwapulumutsa.

5 Zokolola zao anjala azidya, Azitenga ngakhale kuminga, Ndi aludzu ameza cuma cao.

6 Pakuti nsautso siituruka m'pfumbi, Ndi mabvuto saphuka m'nthaka;

7 Koma munthu abadwira mabvuto, Monga mbaliwali zikwera ziuluzika.

8 Koma ine ndikadafuna Mulungu, Ndikadaikira mlandu wanga Mulungu;

9 Amene acita zazikuru ndi zosalondoleka, Zinthu zodabwiza zosawerengeka.

10 Amene abvumbitsa mvula panthaka, Natumiza madzi paminda;

11 Kuika opeputsidwa pamalo ponyamuka, Kuti iwo a maliro akwezedwe posatekeseka.

12 Apititsa pacabe ziwembu za ocenjerera, Kuti manja ao sakhoza kucita copangana cao.

13 Akola eni nzeru m'kucenjerera kwao, Ndi uphungu wa opotoka mtima usonthokera pacabe,

14 Iwo akomana ndi mdima pali dzuwa, Nayambasa dzuwa liri pakati pamtu monga usiku.

15 Apulumutsa aumphawi ku lopanga La kukamwa kwao, ndi ku dzanja la wamphamvu.

16 Potero aumphawi ali naco ciyembekezo, Ndi mphulupulu yatsekedwa pakamwa.

17 Taona, wodala munthu amene Mulungu amdzudzula; Cifukwa cace usapeputsa kulanga kwa Wamphamvuyonse.

18 Pakuti apweteka, namanganso mabala; Alasa, ndi manja ace omwe apoletsa.

19 Adzakupulumutsa m'masautso asanu ndi limodzi; Cinkana mwa asanu ndi awiri palibe coipa cidzakukhudza.

20 Adzakuombola kuimfa m'njala, Ndi ku mphamvu ya lupanga m'nkhondo.

21 Udzabisikira mkwapulo wa lilime, Sudzaciopanso cikadza cipasuko.

22 Cipasuko ndi njala udzaziseka; Ngakhale zirombo za padziko osaziopa.

23 Pakuti udzakhala ndi pangano ndi miyala ya kuthengo; Ndi nyama za kuthengo zidzakhala nawe mumtendere.

24 Ndipo udzapeza kuti pahema pako mpa mtendere; Nudzazonda za m'banja mwako osasowapo kanthu,

25 Udzapezanso kuti mbeu zako zidzacuruka, Ndi obala iwe ngati zitsamba za padziko.

26 Udzafika kumanda utakalamba, Monga abwera nao mtolo wa tirigu m'nyengo yace.

27 Taona, ici tacifunafuna, ciri catero; Ucimvere, nucidziwire wekha.

6

1 Koma Yobu anayankha, nati,

2 Mwenzi atayesa bwino cisoni canga, Ndi kuika matsoka anga pamodzi pamuyeso!

3 Pakuti zikadalemera tsopano koposa mcenga wa kunyanja; Cifukwa cace mau anga ndasonthokera kunena.

4 Pakuti mibvi ya Wamphamvuyonse yandilowa, Mzimu wanga uumwa ulembe wace; Zoopsa za Mulungu zindindandira nkhondo.

5 Kodi mbidzi ilira pokhala nao msipu? Ilira kodi ng'ombe pa cakudya cace?

6 Kodi cinthu cosakolera cidyeka copanda mcere? Coyera ca dzira cikolera kodi?

7 Zimene moyo wanga ukana kuzikhudza Zikunga cakudya cosakolera kwa ine.

8 Ha! ndikadakhala naco cimene ndicipempha, Mulungu akadandipatsa cimene ndicilira!

9 Cimkomere Mulungu kundiphwanya, Alole dzanja lace lindilikhel

10 Pamenepo ndidzasangalala, Ndidzakondwera naco cowawa cosandileka; Pakuti sindinawabisa mau a Woyerayo.

11 Mphamvu yanga njotani kuti ndiyembekeze? Mathedwe anga ndi otani kuti ndipirire?

12 Kodi mphamvu yanga ndiyo mphamvu ya miyala? Mnofu wanga ndi mkuwa kodi?

13 Mulibe thandizo mwa ine ndekha; cipulumutso candithawa.

14 Iye amene akadakomoka, bwenzi lace ayenera kumcitira cifundo; Angaleke kuopa Wamphamvuyonse.

15 Abale anga anacita monyenga ngati kamtsinje, Ngati madzi a timitsinje akupitirira.

16 Amada cifukwa ca madzi oundana. M'menemo cipale cofewa cibisika;

17 Atafikira mafundi, mitsinje iuma; Kukatentha, imwerera m'malo mwao.

18 Aulendo akutsata njira yao apambukapo, Akwerera poti se, natayika.

19 Aulendo a ku Tema anapenyerera, Makamu a ku Seba anaiyembekezera.

20 Anazimidwa popeza adaikhulupirira; Anafikako, nathedwa nzeru.

21 Pakuti tsopano mukhala mamwemo; Muona coopsa, mucitapo mantha.

22 Ngati ndinati, Mundipatse? Kapena, Muperekeko kwa ine cuma canu?

23 Kapena, Mundilanditse m'dzanja la mdani? Kapena, Mundiombole m'dzanja la oopsa?

24 Mundilangize, ndipo ndidzakhala cete ine; Mundizindikiritse umo ndinalakwira.

25 Mau oongoka si ndiwo amphamvu? Koma kudzudzula kwanu mudzudzula ciani?

26 Kodi muyesa kudzudzula mau? Popeza maneno a munthu wodololoka akunga mphepo.

27 Indetu, mugwetsera wamasiye msampha, Mumkumbira bwenzi lanu mbuna.

28 Koma tsopano balindani, mundipenyerere; Ndikanena bodza pamaso panu mudzalizindikira.

29 Bwererani, ndikupemphani, musandiipsire mlandu; Inde, bwereraninso, mlandu wanga ngwolungama.

30 Kodi pali cosalungama palilime panga? Ngati sindizindikira zopanda pace m'kamwa mwanga?

7

1 Kodi munthu alibe nkhondo kunja kuno? Kodi masiku ace sakunga masiku a wolembedwa nchito?

2 Monga kapolo woliralira mthunzi, Monga wolembedwa nchito ayembekezera mphotho yace,

3 Momwemo anandilowetsa miyezi yopanda pace. Nandiikiratu zowawa usiku ndi usiku.

4 Ndigona pansi, ndikuti, Ndidzauka liti? koma usiku undikulira; Ndipo ndimapalapata mpaka mbanda kuca.

5 Mnofu wanga wabvala mphutsi ndi nkanambo zadothi; Khungu langa lang'ambika, nilinyansa.

6 Masiku anga afulumira koposa mphindo ya muomba, Apitirira opanda ciyembekezo.

7 Kumbukila kuti moyo wanga ndiwo mphepo, Diso langa silidzaonanso cokoma.

8 Diso la amene andiona silidzandionanso, Maso ako adzandipenyetsetsa, koma ine palibe.

9 Mtambo wapita watha, Momwemo wakutsikira kumanda sadzakwerakonso.

10 Sadzabweranso ku nyumba yace, Osamdziwanso malo ace.

11 Potero sindidzaletsa pakamwa panga; Ndidzalankhula popsinjika mumzimu mwanga; Ndidzadandaula pakuwawa mtima wanga.

12 Ndine nyanja kodi, kapena cinjoka ca m'nyanja, Kuti Inu mundiikira odikira?

13 Ndikati, Pakama panga mpondisangalatsa, Pogona panga padzacepsa condidandaulitsa;

14 Pamenepo mundiopsa ndi maloto, Nimundicititsa mantha ndi masomphenya;

15 Potero moyo wanga usankha kupotedwa, Ndi imfa, koposa mafupa anga awa.

16 Ndinyansidwa nao moyo wanga; sindidzakhala ndi moyo cikhalire; Mundileke; pakuti masiku anga ndi acabe.

17 Munthu ndani kuti mumkuze, Ndi kuti muike mtima wanu pa iye,

18 Ndi kuti muceze naye m'mawa ndi m'mawa, Ndi kumuyesa nthawi zonse?

19 Mukana kundicokera kufikira liti, Kapena kundileka mpaka nditameza dobvu?

20 Ngati ndacimwa, ndingacitire Inu ciani, Inu wodikira anthu? Mwandiikiranji ndikhale candamali canu? Kuti ndikhale kwa ine ndekha katundu?

21 Mulekeranji kukhululukira kulakwa kwanga ndi kundicotsera mphulupulu yanga? Popeza tsopano ndidzagona kupfumbi; Mudzandifunafuna, koma ine palibe.

8

1 Pamenepo anayankha Bilidadi Msuki, nati,

2 Udzanena izi kufikira liti? Ndipo mau a pakamwa pako adzakhala ngati namondwe kufikira liti?

3 Ngati Mulungu akhotetsa ciweruzo? Ngati Wamphamvuyonse akhotetsa mlandu?

4 Cinkana ana ako anamcimwira Iye, Ndipo anawapereka mwa kulakwa kwao;

5 Koma ukafunitsitsa Mulungu, Ndi kupembedza Wamphamvuyonse;

6 Ukakhala woyera ndi woongoka mtima, Zoonadi adzakugalamukira tsopano, Ndi kupindulitsa pokhala pako polungama.

7 Ndipo cinkana ciyambi cako cinali cacing'ono, Citsiriziro cako cidzacuruka kwambiri.

8 Pakuti ufunsire tsono mbadwo wapitawo, Nusamalire zimene makolo ao adazisanthula;

9 Pakuti ife ndife adzulo, osadziwa kanthu, Popeza masiku athu a pa dziko lapansi ndiwo ngati mthunzi;

10 Amene aja sangakuphunzitse, ndi kukufotokozera, Ndi kuturutsa mau a mumtima mwao?

11 Ngati gumbwa aphuka popanda cinyontho? Ngati mancedza amera popanda madzi?

12 Akali auwisi, sanawaceka, Auma, asanaume mathengo onse ena.

13 Momwemo mayendedwe a onse oiwala Mulungu; Ndi ciyembekezo ca onyoza Mulungu cidzatayika;

14 Kulimbika mtima kwace kudzatyoka, Cikhulupiriro cace cikunga nyumba ya tandaude.

15 Adzatsamira nyumba yace, koma yosamlimbira; Adzaiumirira koma yosakhalitsa.

16 Akhala wamuwisi pali dzuwa, Ndi nthambi zace ziturukira pamunda pace.

17 Mizu yace iyangayanga pa kasupe wamadzi, Apenyerera pokhalapo miyala.

18 Akamuononga kumcotsa pamalo pace, Padzamkana, ndi kuti, Sindinakuona.

19 Taona, ici ndico comkondweretsa panjira pace, Ndi panthaka padzamera ena.

20 Taona, Mulungu sakana munthu wangwiro; Kapena kugwiriziza ocita zoipa.

21 Koma adzadzaza m'kamwa mwako ndi kuseka, Ndi milomo yako kupfuula.

22 Iwo akudana nawe adzabvala manyazi; Ndi hema wa oipa adzakhala kuli zi.

9

1 Pamenepo Yobu anayankha, nati,

2 Zoona, ndidziwa kuti ciri cotero. Koma munthu adzakhala walungama bwanji kwa Mulungu?

3 Akafuna Iye kutsutsana naye, Sadzambwezera Iye mau amodzi onse mwa cikwi.

4 Ndiye wa mtima wanzeru, ndi wa mphamvu yaikuru; Ndaniyo anadziumitsa mtima pa Iye, nakhala nao mtendere?

5 Ndiye amene asuntha mapiri, osacidziwa iwo, Amene amagubuduza mu mkwiyo wace.

6 Amene agwedeza dziko lapansi licoke m'malo mwace, Ndi mizati yace injenjemere.

7 Amene alamulira dzuwa ndipo silituruka, Nakomera nyenyezi cizindikilo cakuzitsekera.

8 Woyala thambo yekha, Naponda pa mafunde a panyanja.

9 Wolenga Mlalang'amba, Akamwiniatsatana, ndi Nsangwe, Ndi Kumpotosimpita,

10 Wocita zazikuru zosasanthulika, Ndi zodabwiza zosawerengeka,

11 Taona, Mulungu apita pali ine, koma sindimpenya; Napitirira, koma osamaindikira ine.

12 Taona, akwatula, adzambwezetsa ndani? Adzanena naye ndani, Mulikucita ciani?

13 Mulungu sadzabweza mkwiyo wace; Athandizi odzikuza awerama pansi pa Iye.

14 Nanga ine tsono ndidzamyankha bwanji, Ndi kusankha mau anga akutsutsana ndi Iye?

15 Ameneyo, cinkana ndikadakhala wolungama, sindikadamyankha; Ndikadangompembedza wondiweruza ine.

16 Ndikadaitana, ndipo akadayankha Iye, Koma sindikadakhulupirira kuti Iye wamvera mau anga,

17 Pakuti andityola ndi mkuntho, Nacurukitsa mabala anga kopanda cifukwa.

18 Sandilola kuti ndipume, Koma andidzaza ndi zowawa.

19 Tikanena za mphamvu, si ndiye wamphamvu? Tikanena za kuweruza, adzamuitana ndani?

20 Cinkana ndikhala wolungama, pakamwa panga padzanditsutsa; Cinkana ndikhala wangwiro, padzanditsutsa wamphulupulu.

21 Cinkana ndikhala wangwiro, sindidzisamalira mwini, Ndipeputsa moyo wanga.

22 Kuli cimodzimodzi monsemo, m'mwemo ndikuti Iye aononga wangwiro ndi woipa pamodzi.

23 Mkwapulo ukapha modzidzimutsa, Adzaseka tsoka la wosacimwa.

24 Dziko lapansi laperekedwa m'dzanja la woipa; Aphimba maso a oweruza ace. Ngati sindiye, pali yaninso?

25 Tsopano masiku anga afulumira kuposa wamtokoma; Athawa osaona cokoma.

26 Apitirira ngati zombo zaliwiro; Ngati mphungu igudukira cakudya cace.

27 Ndikati, Ndidzaiwala condidandaulitsa, Ndidzasintha nkhope yanga yacisoni, ndidzasekerera;

28 Pamenepo ndiopa zisoni zanga zonse, Ndidziwa kuti simudzandiyesa wosacimwa.

29 Mlandu udzanditsutsa; Potero ndigwire nchito cabe cifukwa ninji?

30 Ndikasamba madzi a cipale cofewa Ndi kuyeretsa manja anga ndi sopo;

31 Mudzandibviikanso muli zoola, Ndi zobvala zanga zidzanyansidwa nane.

32 Pakuti sindiye munthu, monga ine, kuti ndimyankhe, Kuti tikomane mlandu.

33 Palibe wakutiweruza, Wakutisanjika ife tonse awiri manja ace.

34 Andicotsere ndodo yace, Coopsa cace cisandicititse mantha;

35 Kuti ndinene, osamuopa, Pakuti sinditero monga umo ndiri.

10

1 Mtima wanga ulema nao moyo wanga, Ndidzadzilolera kudandaula kwanga, Ndidzalankhula pakuwawa mtima wanga.

2 Ndidzati kwa Mulungu, Musanditsutse; Mundidziwitse cifukwa ca kutsutsana nane.

3 Cikukomerani kodi kungosautsa, Kuti mupeputsa nchito yolemetsa manja anu, Ndi kuti muwalira pa uphungu wa oipa?

4 Muli nao maso a thupi kodi? Mupenya kodi monga umo apenyera munthu?

5 Masiku anu akunga masiku a munthu kodi, Zaka zanu zikunga masiku a munthu;

6 Kuti mufunsa mphulupulu yanga, Ndi kulondola coipa canga;

7 Cinkana mudziwa kuti sindiri woipa, Ndipo palibe wakupulumutsa m'dzanja lanu?

8 Manja anu anandiumba, nandiulunga monsemu, Koma mufuna kundiononga.

9 Mukumbukile kuti mwandiumba ngati dothi; Ndipo kodi mudzandibwezera kupfumbi?

10 Simunanditsanula kodi ngati mkaka, Ndi kundilimbitsa ngati mase?

11 Munandibveka khungu ndi mnofu, Ndi kundilumikiza mafupa ndi mitsempha,

12 Mwandipatsa moyo, ndi kundikomera mtima, Ndi masamalidwe anu anasunga mzimu wanga.

13 Koma izi munazibisa mumtima mwamu; Ndidziwa kuti ici muli naco:

14 Ndikacimwa mundipenya; Ndipo simudzandimasula mphulupulu yanga.

15 Ndikakhala woipa, tsoka ine; Ndikakhala wolungama, sindidzakweza mutuwanga; Ndadzazidwa ndi manyazi, Koma penyani kuzunzika kwanga.

16 Ndipo mutu wanga ukadzikweza, mundisaka ngati mkango; Mubweranso ndi kudzionetsera modabwiza kwa ine.

17 Mundikonzeranso mboni zonditsutsa, Ndi kundicurukitsira mkwiyo wanu; Nkhondo yobwereza-bwereza yandigwera.

18 Potero munandibadwitsa cifukwa ninji? Mwenzi nditapereka moyo wanga, lisanandione diso.

19 Ndikadakhala monga ngati sindikadakhala; Akadanditenga pobadwapo kumka nane kumanda.

20 Masiku anga satsala owerengeka nanga? lindani, Bandilekani kuti nditsitsimuke pang'ono,

21 Ndisanacoke kumka kumene sindikabweranso, Ku dziko la mdima ndi la mthunzi wa imfa;

22 Dziko la mdima bii ngati mdima wandiweyani, Dziko la mthunzi wa imfa losalongosoka, Kumene kuunika kukunga mdima.

11

1 Pamenepo anayankha Zofari wa ku Naama, nati,

2 Kodi mau ocurukawa sayenera kuwayankha? Ndi munthu wa milomo ayenera kuyesedwa wolungama?

3 Kodi zotamanda zako ziwatseke anthu pakamwa? Useka kodi, wopanda munthu wakukucititsapo manyazi?

4 Pakuti unena, Ciphunzitso canga ncoona, Ndipo ndiri woyera pamaso pako.

5 Koma, hal mwenzi atanena Mulungu, Ndi kukutsegulira milomo yace motsutsa;

6 Nakufotokozere zinsinsi za nzeru, Popeza zipindika-pindika macitidwe ao! Cifukwa cace dziwa kuti Mulungu akuiwalira mphulupulu zina.

7 Kodi ukhoza kupeza Mulungu mwa kufunafuna? Ukhoza kupeza Wamphamvuyonse motsindika?

8 Kumpeza kutalika ngati kumwamba, ungacitenji? Kuzama ngati kumanda, ungadziwenji?

9 Muyeso wace utalikira utali wace wa dziko lapansi, Citando cace ciposa ca nyanja.

10 Akapita, nakatsekera, Nakaturutsa bwalo la mlandu, adzamletsa ndani?

11 Pakuti adziwa anthu opanda pace, Napenyanso mphulupulu, ngakhale saisamalira.

12 Koma munthu wopanda pace asowa nzeru, Ngakhale munthu abadwa ngati mwana wa mbidzi.

13 Ukakonzeratu mtima wako, Ndi kumtambasulira Iye manja ako;

14 Mukakhala mphulupulu m'dzanja lako, uicotseretu kutali, Ndi cisalungamo cisakhale m'mahema mwako;

15 Popeza pamenepo udzakweza nkhope yako opanda banga; Nudzalimbika osacita mantha;

16 Pakuti udzaiwala cisoni cako, Udzacikumbukila ngati madzi opita;

17 Ndipo moyo wako udzayera koposa usana; Kungakhale kuli mdima kudzakhala ngati m'mawa.

18 Ndipo udzalimbika mtima popeza pali ciyembekezo; Nudzafunafuna, ndi kugona mosatekeseka,

19 Inde udzagona pansi, wopanda wina wakukunjenjemeretsa, Ndipo ambiri adzakupembedza,

20 Koma maso a oipa adzagoma, Ndi pothawirapo padzawasowa, Ndipo ciyembekezo cao ndico kupereka mzimu wao.

12

1 Pamenepo Yobu anayankha, nati,

2 Zoonadi inu ndinu anthu, Ndi nzeru idzafa pamodzi ndi inu.

3 Koma inenso ndiri nayo nzeru monga inu. Sindingakucepereni; Ndani sadziwa zonga izi?

4 Ndine ngati munthu wosekedwa ndi mnansi wace, Ndinaitana kwa Mulungu, ndipo anandiyankha; Munthu wolungama wangwiro asekedwa.

5 Munthu wosatekeseka apeputsa tsoka mumtima mwace, Limlindira woterereka mapazi ace.

6 Mahema a acifwamba akhala mumtendere, Ndi iwo oputa Mulungu alimbika mtima: Amene Mulungu amadzazira dzanja lao.

7 Tafunsira tsono kwa nyamazo, zidzakulangiza, Ndi mbalame za m'mlengalenga, zidzakuuza;

8 Kapena ulankhule ndi dziko lapansi, lidzakulangiza; Ndi nsomba za kunyanja, zidzakufotokozera,

9 Ndaniyo sadziwa nazo izi zonse; Kuti dzanja la Yehova licita ici?

10 M'dzanja mwace muli mpweya wa zamoyo zonse, Ndi mzimu wa munthu ali yense.

11 M'khutumu simuyesa mau, Monga m'kamwa mulawa cakudya cace?

12 Kwa okalamba kuli nzeru, Ndi kwa a masiku ocuruka luntha.

13 Kwa Iye kuli nzeru ndi mphamvu; Uphungu ndi luntha ali nazo.

14 Taona, agamula, ndipo palibe kumanganso; Amtsekera munthu, ndipo palibe kumtsegulira,

15 Taona atsekera madzi, naphwa; Awatsegulira, ndipo akokolola dziko lapansi.

16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi nzeru. Wonyengedwa ndi wonyenga yemwe ali ace.

17 Apita nao maphungu atawafunkhira, Napulukiritsa oweruza milandu.

18 Amasula comangira ca mafumu, Nawamangira nsinga m'cuuno mwao.

19 Apita nao, ansembe atawafunkhica, Nagubuduza amphamvu.

20 Amcotsera wokhulupirika kunena kwace. Nalanda luntha la akulu.

21 Atsanulira mnyozo pa akalonga, Nawasezera olimba lamba lao.

22 Abvumbulutsa zozama mumdima, Naturutsa mthunzi wa imfa ukhale poyera;

23 Acurukitsa amitundu, nawaononganso; Abalalikitsa amitundu, nawabwezanso.

24 Awacotsera akulu a anthu a padziko mtima wao, Nawasokeretsa m'cipululu copanda njira.

25 Iwo ayambasa mumdima mopanda kuunika, Ndipo awayendetsa dzandi dzandi.

13

1 Taonani; diso langa laciona conseci; M'khutu mwanga ndacimva ndi kucizindikira.

2 Cimene mucidziwa inu, inenso ndicidziwa; Sindikuceperani.

3 Koma ine ndidzanena ndi Wamphamvuyonse, Ndipo ndifuna kudzikanira kwa Mulungu.

4 Koma inu ndinu opanga zabodza, Asing'anga opanda pace inu nonse.

5 Mwenzi mutakhala cete konse, Ndiko kukadakhala nzeru zanu.

6 Tamvani tsono kudzikanira kwanga, Tamverani kudzinenera kwa milomo yanga.

7 Kodi munenera Mulungu mosalungama, Ndi kumnenera Iye monyenga?

8 Kodi mukhalira kumodzi ndi Iye? Mundilimbirana mwa Mulungu.

9 Ncokoma kodi kuti Iye akusanthuleni? Kodi mudzamnyenga Iye monga munyenga munthu?

10 Adzakudzudzulani ndithu, Mukacita tsankhu m'tseri.

11 Ukulu wace sukucititsani mantha, Ndi kuopsa kwace sikukugwerani kodi?

12 Zikumbutso zanu ndizo miyambi ya mapulusa; Zodzikanira zanu zikunga malinga adothi.

13 Khalani cete, ndilekeni, kuti ndinene, Condifikira cifike.

14 Ndilumirenji mnofu wanga pamano panga, Ndi kupereka moyo wanga m'dzanja langa?

15 Angakhale andipha koma ndidzamlindira; Komanso ndidzaumirira mayendedwe anga pamaso pace.

16 Iye adzakhalanso cipulumutso canga, Pakuti wonyoza Mulungu sadzafika pamaso pace.

17 Mvetsetsani mau anga, Ndi kunenetsa kwanga kumveke m'makutu mwanu.

18 Taonani tsono, ndalongosola mlandu wanga; Ndidziwa kuti adzandimasula ndiri wolungama,

19 Ndaniyo adzatsutsana nane? Ndikakhala cete, ndidzapereka mzimu wanga.

20 Zinthu ziwiri zokha musandicitire, Pamenepo sindidzabisalira nkhope yanu:

21 Mundicotsere dzanja lanu kutali, Ndi kuopsa kwanu kusandicititse mantha.

22 Pamenepo muitane, ndipo ndidzayankha; Kapena ndinene ndine, ndipo mundiyankhe ndinu.

23 Mphulupulu zanga ndi zocimwa zanga ndi zingati? Mundidziwitse kulakwa kwanga ndi cimo langa,

24 Mubisiranji nkhope yanu, Ndi kundiyesa mdani wanu?

25 Kodi mudzaopsa tsamba lakungouluka, Ndi kulondola ziputu zouma?

26 Pakuti mundilembera zinthu zowawa, Ndi kundipatsa ngati colowa mphulupulu za ubwana wanga.

27 Mulonganso mapazi anga m'zigologolo, ndi kupenyerera mayendedwe anga onse; Mudzilembera malire mopanika mapazi anga;

28 Momwemo munthu akutha ngati cinthu coola, Ngati cobvala codyedwa ndi numbi

14

1 Munthu wobadwa ndi mkazi Ngwa masiku owerengeka, nakhuta mabvuto,

2 Aturuka ngati duwa, nafota; Athawa ngati mthunzi, osakhalitsa.

3 Ndipo kodi mumtsegulira maso anu wotereyo, Ndi kunditenga kunena nane mlandu Inu?

4 Adzaturutsa coyera m'cinthu codetsa ndani? nnena mmodzi yense.

5 Popeza masiku ace alembedwa, ciwerengo ca miyezi yace cikhala ndi Inu, Ndipo mwamlembera malire ace, kuti asapitirirepo iye;

6 Mumleke osamthira maso, kuti apumule, Kuti akondwere nalo tsiku lace monga wolembedwa nchito.

7 Pakuti akaulikha mtengo pali ciyembekezo kuti udzaphukanso, Ndi kuti nthambi yace yanthete siidzasowa.

8 Ngakhale muzu wace wakalamba m'nthaka, Ndi tsinde lace likufa pansi;

9 Koma pa mnunkho wa madzi udzaphuka, Nudzaswa nthambi ngati womera.

10 Koma munthu akufa atacita liondeonde Inde, munthu apereka mzimu wace, ndipo ali kuti?

11 Madzi acoka m'nyanja, Ndi mtsinje ukuphwa, nuuma;

12 Momwemo munthu agona pansi, osaukanso; Kufikira miyamba kulibe, sadzaukanso, Kapena kuutsidwa pa tulo tace.

13 Ha! mukadandibisa kumanda, Mukadandisunga m'tseri, mpaka wapita mkwiyo wanu. Mukadandiikira nthawi, ndi kundikumbukira.

14 Atafa munthu, adzakhalanso ndi moyo kodi? Ndikadayembekeza masiku onse a nkhondo yanga, Mpaka kwafika kusandulika kwanga,

15 Mukadaitana, ndipo ndikadakuyankhani; Mukadakhumba nchito ya manja anu.

16 Koma tsopano muwerenga maponda mwanga; Kodi simuyang'anitsa cimo langa?

17 Colakwa canga caikidwa m'thumba lokomedwa cizindikilo; Ndipo mumanga pamodzi mphulupulu zanga.

18 Ndipo zoonadi, likagwa phiri, latha; Ndi thanthwe lisunthika m'malo mwace;

19 Madzi anyenya miyala; Zosefukira zao zikokolola pfumbi la nthaka; Ndipo muononga ciyembekezo ca munthu.

20 Mumlaka cilakire, napita iye; Musintha nkhope yace, mumuuza acoke.

21 Ana ace aona ulemu osadziwa iye; Napeputsidwa, koma osazindikira za iwo.

22 Koma thupi lace limuwawira yekha, Ndi mtima wace umliritsa yekha.

15

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha, nati,

2 Kodi mwini nzeru ayankhe ndi kudziwa kouluzika, Ndi kudzaza mimba yace ndi mphepo ya kum'mawa?

3 Kodi atsutsane ndi mnzace ndi mau akusathandiza? Kapena ndi maneno akusaphindulitsa?

4 Zedi uyesa cabe mantha, Nucepsa cilingiriro pamaso pa Mulungu.

5 Pakuti pakamwa pako paphunzitsa mphulupulu zako, Nusankha lilime la ocenjerera.

6 Pakamwa pako pakutsutsa, si ine ai. Inde milomo yako ikucitira umboni wakukutsutsa.

7 Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kapena unayamba kulengedwa ndiwe, osati mapiri?

8 Kodi unamva uphungu wacinsinsi wa Mulungu? Ndipo unadzikokera nzeru kodi?

9 Udziwa ciani, osacidziwa ife? Uzindikira ciani, cosakhala mwa ife?

10 Pakati pa ife pali aimvi, ndi okalambitsa, Akuposa atate wako masiku ao,

11 Masangalatso a Mulungu akucepera kodi? Kapena uli naco cinsinsi kodi?

12 Mtima wako usonthokeranji nawe? Maso ako aphethira-phethira cifukwa ninji?

13 Kuti utembenuza mzimu wako utsutsane ndi Mulungu, Ndi kulola mau otere aturuke m'kamwa mwako.

14 Munthu nciani kuti akhale woyera, Wobadwa ndi mkazi kuti akhale wolungama?

15 Taona, Mulungu sakhulupirira opatulika ace; Ngakhale m'mwamba simuyera pamaso pace,

16 Koposa kotani nanga munthu wonyansa ndi wodetsa, Wakumwa cosalungama ngati madzi.

17 Ndidzakuonetsa, undimvere; Cimene ndinaciona, ndidzakufotokozera;

18 Cimene adacinena anzeru, Adacilandira kwa makolo ao, osacibisa;

19 Ndiwo amene analandira okha dzikoli, Wosapita mlendo pakati pao;

20 Munthu woipa adzipweteka masiku ace onse, Ndi zaka zowerengeka zisingikira woopsa.

21 M'makutu mwace mumveka zoopsetsa; Pali mtendere amfikira wakumuononga.

22 Sakhulupirira kuti adzaturukamo mumdima, Koma kuti lupanga limlindira;

23 Ayendayenda ndi kufuna cakudya, nati, Ciri kuti? Adziwa kuti lamkonzekeratu pafupi tsiku lamdima,

24 Nsautso ndi cipsinjo zimcititsa mantha, Zimlaka ngati mfumu yokonzekeratu kunkhondo;

25 Pakuti amtambasula dzanja lace moyambana ndi Mulungu, Napikisana ndi Wamphamvuyonse.

26 Amthamangira Iye mwaliuma, Ndi zikopa zace zocindikira.

27 Popeza anakuta nkhope yace ndi kunenepa kwace, Nacita mafunyenye a mafuta m'zuuno zace;

28 Adzakhala m'midzi yopasuka, M'nyumba zosakhalamo munthu, Zoti zisandulika muunda.

29 Sadzakhala wolemera, ndi cuma cace sicidzakhalitsa, Ndi zipatso zace sizidzacuruka padziko.

30 Sadzacoka mumdima; Lawi la moto lidzaumitsa nthambi zace; Ndipo adzacoka ndi mpumo wa m'kamwa mwace.

31 Asatame zopanda pace, kudzinyenga nazo; Pakuti zopanda pace zidzakhala combwezera cace.

32 Cidzacitika isanadze nthawi yace; Pakuti nthambi yace siidzaphuka.

33 Adzayoyoka zipatso zace zosapsa ngati mpesa, Nadzathothoka maluwa ace ngati mtengo wazitona.

34 Pakuti msonkhano wa onyoza Mulungu udzakhala cumba, Ndi moto udzapsereza mahema a olandira cokometsera mlandu.

35 Aima ndi cobvuta, nabala mphulupulu, Ndi m'mimba mwao mukonzeratu cinyengo.

16

1 Pamenepo Yobu anayankha, nati,

2 Ndamva zambiri zotere; Inu nonse ndinu otonthoza mtima mondilemetsa.

3 Kodi adzatha mau ouluzika? Kapena cikuwindula nciani kuti uyankha zotere?

4 Inenso ndikadanena monga inu, Moyo wanu ukadakhala m'malo mwa moyo wanga, Ndikadalumikizanitsa mau akutsutsana nanu, Ndi kukupukusirani mutu wanga.

5 Koma ndikadakulimbikitsani ndi m'kamwa mwanga, Ndi citonthozo ca milomo yanga cikadatsitsa cisoni canu.

6 Cinkana ndinena cisoni canga sicitsika; Ndipo ndikaleka, cindicokera nciani?

7 Koma tsopano wandilemetsa Iye; Mwapasula msonkhano wanga wonse.

8 Kundigwira kwanu, ndiko umboni wonditsutsa, Kuonda kwanga kundiukira, kucita umboni pamaso panga.

9 Iye ananding'amba m'kundida kwace, nakwiya nane, Anandikukutira mano; Mdani wanga ananditong'olera maso ace.

10 Iwo anandiyasamira pakamwa pao; Anandiomba pama ndi kunditonza; Asonkhana pamodzi kunditsutsa.

11 Mulungu andipereka kwa osalungama, Nandiponya m'manja a oipa.

12 Ndinali mkupuma, koma anandityola; Inde anandigwira pakhosi, nandiphwanya; Anandiimika ndikhale candamali.

13 Eni mauta ace andizinga, Ang'amba imso zanga, osazileka; Natsanulira pansi ndulu yanga.

14 Andipasula-pasula; Andithamangira ngati wamphamvu.

15 Ndadzisokerera ciguduli ku khungu langa, Ndipo ndaipsa mphamvu yanga m'pfumbi.

16 Nkhope yanga njodetsedwa ndi kulira misozi, Ndi pa zikope zanga pali mthunzi wa imfa;

17 Pangakhale palibe ciwawa m'manja mwanga, Ndi pemphero langa ndi loyera.

18 Dziko iwe, usakwirire mwazi wanga, Ndi kulira kwanga kusowe popumira.

19 Tsopanonso, taona, mboni yanga iri kumwamba, Ndi nkhoswe yanga ikhala m'mwamba.

20 Mabwenzi anga andinyoza; Koma diso langa lilirira misozi kwa Mulungu;

21 Ha! munthu akadapembedzera mnzace kwa Mulungu, Monga munthu apembedzera mnansi wace!

22 Pakuti zitafika zaka zowerengeka, Ndidzamuka ku njira imene sindibwererako.

17

1 Mzimu wanga watha, masiku anga afafanizika, Kumanda kwandikonzekeratu.

2 Zoonadi, ali nane ondiseka; Ndi diso langa liri cipenyere m'kundiwindula kwao.

3 Mupatse cigwiriro tsono, mundikhalire cikole Inu nokha kwanu; Ndani adzapangana nane kundilipirira?

4 Pakuti mwabisira mtima wao nzeru; Cifukwa cace simudzawakuza.

5 Iye wakupereka mabwenzi ace kuukapolo, M'maso mwa ana ace mudzada.

6 Anandiyesanso nthanthi za anthu; Ndipo ndakhala ngati munthu womthira malobvu pankhope pace.

7 M'diso mwanga mucita cizirezire cifukwa ca cisoni, Ndi ziwalo zanga zonse ziribe cithunzi.

8 Anthu oongoka mtima adzadabwa naco, Ndi munthu wosalakwa adzadziutsa kumtsotsa wonyoza Mulunguyo.

9 Koma wolungama asungitsa njira yace, Ndi iye wa manja oyera adzakulabe mumphamvu.

10 Koma bwerani inu nonse, idzani tsono; Pakuti sindipeza mwa inu wanzeru.

11 Masiku anga apitirira, zolingirira zanga zaduka, Zace zace zomwe za mtima wanga.

12 Zisanduliza usiku ukhale usana; Kuunika kuyandikana ndi mdima.

13 Ndikayembekezera kumanda kukhale nyumba yanga; Ndikayala pogona panga mumdima.

14 Ndikati kwa dzenje, Ndiwe atate wanga; Kwa mphutsi, Ndiwe mai wanga ndi mlongo wanga;

15 Ciri kuti ciyembekezo canga? Inde, ciyembekezo canga adzaciona ndani?

16 Cidzatsikira ku mipingiridzo ya kumanda, Pamene tipumulira pamodzi kupfumbi.

18

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha, nati,

2 Musaka mau kufikira liti? Zindikirani, ndi pamenepo tidzanena.

3 Tiyesedwa bwanji ngati nyama za kuthengo, Ndi kukhala odetsedwa pamaso panu?

4 Iwe wodzing'amba mumkwiyo mwako, Kodi dziko lapansi lisiyidwe cifukwa ca iwe? Kapena thanthwe lisunthike m'malo mwace?

5 Inde, kuunika kwa woipa kudzazima, Ndi lawi la moto wace silidzawala.

6 Kuunikaku kudzada m'hema mwace, Ndi nyali yace ya pamwamba pace idzazima.

7 Mapondedwe ace amphamvu adzasautsidwa, Ndi uphungu wace wace udzamgwetsa.

8 Pakuti aponyedwa m'ukonde ndi mapazi ace, Namaponda pamatanda.

9 Msampha udzamgwira kucitende, Ndi khwekhwe lidzamkola.

10 Msampha woponda umbisikira pansi, Ndi msampha wa cipeto panjira.

11 Zoopetsa zidzamcititsa mantha monsemo, Nadzampitikitsa kumbuyo kwace.

12 Njala idzatha mphamvu yace, Ndi tsoka lidzamkonzekeratu pambali pace.

13 Zidzatha ziwalo za thupi lace, Mwana woyamba wa imfa adzatha ziwalo zace.

14 Adzazulidwa kuhema kwace kumene anakhulupirira; Nadzatengedwa kumka naye kwa mfumu ya zoopsa.

15 Adzakhala m'hema mwace iwo amene sali ace; Miyala yasulfure idzawazika pokhala pace.

16 Mizu yace idzauma pansi, Ndi nthambi yace idzafota m'mwamba.

17 Cikumbukilo cace cidzatayika m'dziko, Ndipo adzasowa dzina kukhwalala.

18 Adzamkankha acoke ku kuunika alowe kumdima; Adzampitikitsa acoke m'dziko lokhalamo anthu.

19 Sadzakhala naye mwana kapena cidzukulu mwa anthu amtundu wace, Kapena wina wotsalira kumene anakhalako.

20 Akudza m'mbuyo adzadabwa nalo tsiku lace, Monga aja omtsogolera anagwidwa mantha.

21 Zoonadi, zokhalamo osalungama zitero, Ndi malo a iye amene sadziwa Mulungu ndi awa.

19

1 Koma Yobu anayankha, nati,

2 Mudzasautsa moyo wanga kufikira liti, Ndi kundityolatyola nao mau?

3 Kakumi aka mwandicititsa manyazi; Mulibe manyazi kuti mundiumira mtima.

4 Ndipo ngati ndalakwa ndithu, Kulakwa kwanga kuli ndi ine ndekha.

5 Ngati inu mudzikuza ndithu pa ine, Ndi kundichulira mtonzo wanga kuti munditsutse nao;

6 Dziwani tsopano kuti Mulungu wandikhotetsera mlandu wanga, Nandizinga ndi ukonde wace.

7 Taonani, ndipfuula kuti, Ciwawa! koma sandimvera; Ndikuwa, koma palibe ciweruzo.

8 Iye ananditsekera njira kuti ndisapitireko, Naika mdima poyendapo ine.

9 Anandibvula ulemerero wanga, Nandicotsera korona pamutu panga,

10 Nandigamula ponsepo, ndipo ndamukatu; Nacizula ciyembekezo canga ngati mtengo.

11 Wandiyatsiranso mkwiyo wace, Nandiyesera ngati wina wa adani ace.

12 Ankhondo ace andidzera pamodzi, nandiundira njira yao, Nandimangira misasa pozinga hema wanga.

13 Iye anandicotsera abale anga kutali, Ndi odziwana nane andiyesa mlendo konse.

14 Anansi anga andisowa, Ndi odziwana nane bwino andiiwala.

15 Iwo a m'nyumba mwanga ndi adzakazi anga andiyesa mlendo; Ndine wacilendo pamaso pao.

16 Ndikaitana kapolo wanga, sandibwezera mau, Cinkana ndimpembedza pakamwa panga.

17 Mpweya wanga unyansira mkazi wanga, Cinkana ndinampembedza ndi kuchula ana a thupi langa.

18 Angakhale ana ang'ono andipeputsa, Ndikanyamuka, andinena;

19 Mabwenzi anga eni eni onse anyansidwa nane; Ndi onse ndakondana nao asandulika adani anga.

20 Pfupa langa laumirira pa khungu langa ndi mnofu wanga, Ndipo ndapulumuka ndiri nazo nkhama za mano anga.

21 Ndicitireni cifundo, ndicitireni cifundo, mabwenzi anga inu; Pakuti dzanja la Mulungu landikhudza.

22 Mundilondola bwanji ngati Mulungu, Losakukwanirani thupi langa?

23 Ha! akadalembedwa mau anga! Ha! akadalembedwa m'buku!

24 Akadawazokota pathanthwe cikhalire, Ndi cozokotera cacitsulo ndi kuthira ntobvu!

25 Koma ndidziwa kuti Mombolo wanga ali ndi moyo, Nadzauka potsiriza papfumbi.

26 Ndipo khungu langa litaonongeka, Pamenepo wopanda thupi langa, ndidzapenya Mulungu;

27 Amene ndidzampenya ndekha, Ndi maso anga adzamuona, si wina ai. Imso zanga zatha m'kati mwanga.

28 Mukati, Tiyeni timlondole! Popeza cifukwa ca mlandu capezeka mwa ine;

29 Mucite nalo mantha lupanga; Pakuti mkwiyo utenga zolakwa za lupanga, Kuti mudziwe pali ciweruzo.

20

1 Pamenepo anayankha Zofari Mnaama, nati,

2 M'mwemo zolingirira zanga zindiyankha, Cifukwa cace ndifulumidwa m'kati mwanga.

3 Ndamva kudzudzula kwakundicititsa manyazi, Ndi mzimu wa nzeru yanga undiyankha.

4 Kodi sucidziwa ici ciyambire kale lomwe, Kuyambira anaika munthu pa dziko lapansi,

5 Kuti kupfuula kokondwera kwa woipa sikukhalira kutha, Ndi cimwemwe ca wonyoza Mulungu cikhala kamphindi?

6 Cinkana ukulu wace ukwera kumka kuthambo, Nugunda pamitambo mutu wace;

7 Koma adzatayika kosatha ngati zonyansa zace; Iwo amene adamuona adzati, Ali kuti iye?

8 Adzauluka ngati loto, osapezekanso; Nadzaingidwa ngati masomphenya a usiku.

9 Diso lidamuonalo silidzamuonanso; Ndi malo ace sadzampenyanso.

10 Ana ace adzapempha aumphawi awakomere mtima; Ndi manja ace adzabweza cuma cace.

11 Mafupa ace adzala nao unyamata wace, Koma udzagona naye pansi m'pfumbi.

12 Cinkana coipa cizuna m'kamwa mwace, Cinkana acibisa pansi pa lilime lace;

13 Cinkana acisunga, osacileka, Naoikhalitsa m'kamwa mwace;

14 Koma cakudya cace cidzasandulika m'matumbo mwace, Cidzakhala ndulu ya mphiri mkati mwace.

15 Anacimeza cuma koma adzacisanzanso; Mulungu adzaciturutsa m'mimba mwace.

16 Adzayamwa ndulu ya mphiri; Pakamwa pa njoka padzamupha.

17 Sadzapenyerera timitsinje, Toyenda nao uci ndi mafuta.

18 Cimene adagwiriraco nchito, adzacibweza, osacimeza; Sadzakondwera monga mwa zolemera zace adaziona.

19 Pakuti anapsinja, nasiya aumphawi; Analanda nyumba mwaciwawa, imene sanaimanga.

20 Popeza sanadziwa kupumula m'kati mwace, Sadzalanditsa kanthu ka zofunika zace.

21 Sikunatsalira kanthu kosadya iye, Cifukwa cace zokoma zace sizidzakhalitsa.

22 Pomkwanira kudzala kwace adzakhala m'kusauka; Dzanja la yense wobvutika lidzamgwera,

23 Poti adzaze mimba yace, Mulungu adzamponyera mkwiyo wace waukali, Nadzambvumbitsira uwu pakudya iye.

24 Adzathawa cida cacitsulo, Ndi mubvi wa uta wamkuwa udzampyoza.

25 Auzula, nuturuka m'thupi mwace; Inde nsonga yonyezimira ituruka m'ndulu mwace; Zamgwera zoopsa.

26 Zamdima zonse zimsungikira zikhale cuma cace, Moto wosaukoleza munthu udzampsereza; Udzatha wotsalira m'hema mwace.

27 M'mwamba mudzabvumbulutsa mphulupulu yace, Ndi dziko lapansi lidzamuukira.

28 Phindu la m'nyumba mwace lidzacoka, Akatundu ace adzamthawa tsiku la mkwiyo wace.

29 Ili ndi gawo la munthu woipa, locokera kwa Mulungu, Ndi colowa amuikiratu Mulungu.

21

1 Pamenepo Yobu anayankha, nati,

2 Mvetsetsani mau anga; Ndi ici cikhale citonthozo canu.

3 Mundilole, ndinene nanenso; Ndipo nditanena ine, sekani.

4 Kodi ine, kudandaula kwanga, ndidandaulira munthu? Ndipo ndilekerenji kupsa mtima?

5 Ndiyang'anireni, nimusumwe, Gwirani pakamwa panu.

6 Ndikangokumbukila ndibvutika mtima, Ndi thupi langa licita nyau nyau.

7 Oipa akhaliranji ndi moyo, Nakalamba, nalemera kwakukuru?

8 Mbeu zao zikhazikika pamodzi nao pankhope pao, Ndi ana ao pamaso pao,

9 Nyumba zao sizitekeseka ndi mantha, Ngakhale ndodo ya Mulungu siiwakhalira.

10 Ng'ombe yao yamphongo imakwera, yosakanika; Ng'ombe yao yaikazi imaswa, yosapoloza.

11 Aturutsa makanda ao ngati gulu, Ndi ana ao amabvinabvina.

12 Ayimbira lingaka ndi zeze, Nakondwera pomveka citoliro.

13 Atsekereza masiku ao ndi zokoma, Natsikira m'kamphindi kumanda.

14 Koma adati kwa Mulungu, Ticokereni; Pakuti sitifuna kudziwa njira zanu.

15 Wamphamvuyonse ndiye yani kuti timtumikire? Ndipo tidzapindulanji pakumpemphera Iye?

16 Taonani, zokoma zao siziri m'dzanja lao; (Koma uphungu wa oipa unditalikira.)

17 Ngati nyali za oipa zizimidwa kawiri kawiri? Ngati tsoka lao liwagwera? Ngati Mulungu awagawira zowawa mu mkwiyo wace?

18 Ngati akunga ziputu zomka ndi mphepo, Ngati mungu wouluzika ndi nkuntho?

19 Mukuti, Mulungu asungira ana ace a munthu coipa cace, Ambwezere munthuyo kuti acidziwe.

20 Aone yekha cionongeko cace m'maso mwace, Namwe mkwiyo wa Wamphamvuyonse.

21 Pakuti comsamalitsa nyumba yace nciani, atapita iye, Ciwerengo ca miyezi yace citadulidwa pakati?

22 Ngati pali munthu wakumphunzitsa Mulungu nzeru? Popeza Iye aweruza mlandu iwo okwezeka.

23 Wina akufa, wabiriwiri, Ali cikhalire ndi cipumulire.

24 Mbale zace zidzala ndi mkaka; Ndi wongo wa m'mafupa ace uli momwe.

25 Koma mnzace akufa ali nao mtima wakuwawa, Osalawa cokoma konse.

26 Iwo agona cimodzimodzi kupfumbi, Ndi mphutsi ziwakuta.

27 Taonani, ndidziwa maganizo anu, Ndi ciwembu mundilingirira moipa,

28 Pakuti munena, Iri kuti nyumba ya kalonga? Ndi hema wokhalamo woipa ali kuti?

29 Simunawafunsa kodi opita m'njira? Ndipo simusamalira zotsimikiza zao?

30 Zakuti munthu woipa asungika tsiku la tsoka? Naturutsidwa tsiku la mkwiyo?

31 Adzamfotokozera ndani njira yace pamaso pace? Nadzamlipitsa ndani pa ici anacicita?

32 Potsiriza pace adzapita naye kumanda, Nadzadikira pamanda pace,

33 Zibuma za kucigwa zidzamkomera. Adzakoka anthu onse amtsate, Monga anamtsogolera osawerengeka.

34 Potero munditonthozeranji nazo zopanda pace, Popeza m'mayankho mwanu mutsala mabodza okha?

22

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha, nati,

2 Kodi munthu apindulira Mulungu? Koma wanzeru angodzipindulira yekha.

3 Kodi Wamphamvuyonse akondwera nako kuti iwe ndiwe wolungama? Kapena kodi apindula nako kuti ukwaniritsa njira zako?

4 Kodi akudzudzula, nadza nawe kumlandu, Cifukwa ca kumuopa kwako?

5 Zoipa zako sizicuruka kodi? Ndi mphulupulu zako sizikhala zosawerengeka kodi?

6 Pakuti wamtenga cikole kwa mbale wako wopanda cifukwa, Ndi kubvula ausiwa zobvala zao.

7 Sunampatsa wolema madzi amwe, Ndi wanjala unammana cakudya.

8 Koma munthu mwini mphamvu, dziko ndi lace; Ndi munthu wobvomerezeka, anakhala momwemo.

9 Unabweza akazi amasiye osawaninkha kanthu, Ndi manja a ana amasiye anatyoledwa.

10 Cifukwa cace misampha ikuzinga. Ndi mantha akubvuta modzidzimutsa,

11 Kapena mdima kuti ungaone, Ndi madzi aunyinji akumiza.

12 Kodi Mulungu sakhala m'mwamba m'tali? Ndipo penyani kutalika kwace kwa nyenyezi, ziri m'talitali.

13 Ndipo ukuti, Adziwa ciani Mulungu? Aweruza kodi mwa mdima wa bii?

14 Mitambo ndiyo comphimba, kuti angaone; Ndipo amayenda pa thambo lakumwamba.

15 Udzasunga kodi njira yakale, Anaiponda anthu amphulupulu?

16 Amene anakwatulidwa isanafike nyengo yao, Cigumula cinakokolola kuzika kwao;

17 Amene anati kwa Mulungu, Ticokereni; Ndipo, Angaticitire ciani Wamphamvuyonse?

18 Angakhale Iye adadzaza nyumba zao ndi zabwino; Koma uphungu wa oipa unditalikira.

19 Olungama aciona nakondwera; Ndi osalakwa awaseka pwepwete,

20 Ndi kuti, Zoonadi, otiukirawo alikhidwa, Ndi zowatsalira, moto unazipsereza.

21 Uzolowerane ndi Iye, nukhale ndi mtendere; Ukatero zokoma zidzakudzera,

22 Landira tsono cilamulo pakamwa pace, Nuwasunge maneno ace mumtimamwako.

23 Ukabweranso kwa Wamphamvuyonse, udzamanga bwino; Ukacotsera cosalungama kutali kwa mahema ako.

24 Ndipo utaye cuma cako kupfumbi, Ndi golidi wa ku ofiri ku miyala ya kumitsinje.

25 Ndipo Wamphamvuyonse adzakhala cuma cako, Ndi ndarama zako zofunika.

26 Pakuti pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuyonse, Ndi kuweramutsa nkhope yako kwa Mulungu.

27 Udzampemphera ndipo adzakumvera; Nudzatsiriza zowinda zako.

28 Ukatsimikiza mtima kakuti, kadzakhazikikira iwe; Ndi kuunika kudzawala pa njira zako.

29 Anthu akakugwetsa pansi, udzati, Adzandikweza; Ndipo adzapulumutsa wodzicepetsayo.

30 Adzamasula ngakhale woparamula, Inde adzamasuka mwa kuyera kwa manja ako.

23

1 Koma Yobu anayankha, nati,

2 Lero lomwe kudandaula kwanga kumawawa; Kulanga kwanga kuposa kubuula kwanga m'kulemera kwace.

3 Ha! ndikadadziwa kumene ndikampeza Mulungu, Kuti ndifike ku mpando wace!

4 Ndikadalongosola mlandu wanga pamaso pace, Ndikadadzaza m'kamwa mwanga ndi matsutsano.

5 Ndikadadziwa mau akadandiyankha ine, Ndikadazindikira cimene akadanena nane.

6 Akadatsutsana nane kodi mwa mphamvu yace yaikuru? Iai, koma akadandicherera khutu.

7 Apo woongoka mtima akadatsutsana naye; Ndipo ndikadapulumuka cipulumukire kwa Woweruza wanga.

8 Taonani, ndikamka m'tsogolo, kulibe Iye; Kapena m'mbuyo sindimzindikira;

9 Akacita Iye kulamanzere, sindimpenyerera; Akabisala kulamanja, sindimuona,

10 Koma adziwa njira ndilowayi; Atandiyesa ndidzaturuka ngati golidi.

11 Phazi langa lagwiratu moponda Iye, Ndasunga njira yace, wosapambukamo.

12 Sindinabwerera kusiya malamulo a pa milomo yace; Ndasungitsa mau a pakamwa pace koposa lamulo langa langa.

13 Koma Iye ndiye wa mtima umodzi, adzambweza ndani? Ndi ici cimene moyo wace ucifuna acicita.

14 Pakuti adzacita condiikidwiratu; Ndipo zambiri zotere ziri ndi Iye.

15 Cifukwa cace ndiopsedwa pankhope pace; Ndikalingirira, ndicita mantha ndi Iye.

16 Pakuti Mulungu walefula mtima wanga, Ndi Wamphamvuyonse wandiopsa.

17 Popeza sindinalikhidwa usanafike mdimawo, Ndipo sanandiphimbira nkhope yanga ndi mdima wa bii.

24

1 Wamphamvuyonse alekeranji kuikiratu nyengo? Ndi iwo omdziwa alekeranji kudziwa masiku ace?

2 Alipo akusendeza malire; Alanda gulu la zoweta, nazidyetsa.

3 Akankhizira kwao buru wa amasiye, Atenga ng'ombe ya mfedwa ikhale cikole.

4 Apambukitsa aumphawi m'njira; Osauka a padziko abisala pamodzi.

5 Taonani, ngati mbidzi za m'cipululu Aturukira ku nchito zao, nalawirira nkufuna cakudya; Cipululu ciwaonetsera cakudya ca ana ao.

6 Atema dzinthu zao m'munda; Natola khunkha m'munda wampesa wa woipa.

7 Agona amarisece usiku wonse opanda cobvala, Alibe copfunda pacisanu.

8 Abvumbwa ndi mvula kumapiri, Nafukata thanthwe posowa pousapo.

9 Akwatula wamasiye kubere, Natenga cikole cobvala ca osauka;

10 Momwemo ayenda amarisece opanda cobvala, Nasenza mtolo wa dzinthu ali ndi njala.

11 M'kati mwa malinga a iwo aja ayenga mafuta; Aponda mphesa moponderamo, namva ludzu.

12 M'mudzi waukuru anthu abuula alinkufa; Ndi moyo wa iwo olasidwa upfuula; Koma Mulungu sasamalira coipaco.

13 Iwo ndiwo amene apikisana nako kuunika, Sadziwa njira zace, Sasunga mayendedwe ace.

14 Kukaca auka wambanda, napha wosauka ndi waumphawi; Ndi usiku asanduka mbala.

15 Ndipo diso la wacigololo liyombekezera cisisira, Ndi kuti, Palibe diso lidzandiona; Nabvala cophimba pankhope pace.

16 Kuli mdima aboola nyumba, Usana adzitsekera, Osadziwa kuunika.

17 Pakuti iwo onse auyesa m'mawa mthunzi wa imfa; Pakuti adziwa zoopsa za mthunzi wa imfa.

18 Atengedwa ngati coyandama pamadzi; Gawo lao litembereredwa padziko; Sadzalunjikanso njira ya minda yamphesa.

19 Cirala ndi dzuwa zitha madzi a cipale cofewa, Momwemo manda acita nao ocimwa.

20 M'mimba mudzamuiwala; mphutsi zidzamudya mokondwera. Sadzamkumbukilanso; Ndipo cosalungama cidzatyoledwa ngati mtengo.

21 Alusira cumba wosabala, Osamcitira wamasiye cokoma.

22 Mulungu awakhalitsa amphamvu mwa mphamvu yace; Iwo aukanso m'mene anayesa kuti sadzakhala ndi moyo.

23 Awalola akhale osatekeseka, ndipo alimbikapo; Koma maso ace ali pa njira zao.

24 Akwezeka; m'kamphindi kuti zi; Inde atsitsidwa, acotsedwa monga onse ena, Adutidwa ngati tirigu ngala zace.

25 Ndipo ngati si kutero, anditsutsa ndani kuti ndiri wabodza, Ndi kuyesa mau anga opanda pace?

25

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha, nati,

2 Kulamulira ndi kuopsa kuti ndi Iye; Acita mtendere pa zam'mwamba zace.

3 Ngati awerengedwa makamu ace? Ndipo ndaniyo, kuunika kwace sikumturukira?

4 Potero munthu akhala bwanji wolungama kwa Mulungu? Kapena wobadwa ndi mkazi akhala woyera bwanji?

5 Taonani, ngakhale mwezi ulibe kuwala; Ndi nyenyezi siziyera pamaso pace;

6 Kopambana kotani nanga munthu, ndiye mphutsi! Ndi wobadwa ndi munthu, ndiyo nyongolotsi!

26

1 Koma Yobu anayankha, nati,

2 Wamthandiza bwanji wopanda mphamvu, Kulipulumutsa dzanja losalimba!

3 Wampangira bwanji wopanda nzeruyu! Ndi kudziwitsa nzeru zeni zeni mocurukal

4 Wafotokozera yani mau? Ndi mzimu wa yani unaturuka mwa iwe?

5 Adafawo anjenjemera Pansi pa madzi ndi zokhalamo,

6 Kumanda kuli padagu pamaso pace, Ndi kucionongeko kusowa cophimbako,

7 Ayala kumpoto popanda kanthu, Nalenjeka dziko pacabe.

8 Amanga madzi m'mitambo yace yocindikira; Ndi mtambo sung'ambika pansi pace,

9 Acingira pa mpando wace wacifumu, Nayalapo mtambo wace.

10 Analembera madziwo malire, Mpaka polekeza kuunika ndi mdima.

11 Mizati ya thambo injenjemera, Ndi kudabwa pa kudzudzula kwace.

12 Mwa mphamvu yace agwetsa nyanja bata; Ndipo mwa luntha lace akantha kudzikuza kwace.

13 Mwa mzimu wace anyezimiritsa thambo; Dzanja lace linapyoza njoka yothawayo.

14 Taonani, awa ndi malekezero a njira zace; Ndi cimene tikumva za Iye ndi cinong'onezo cacing'ono; Koma kugunda kwa mphamvu yace akuzindikiritsa ndani?

27

1 Ndipo Yobu anaonjezanso mwambi wace, nati,

2 Pali Mulungu, amene anandicotsera zoyenera ine, Ndi Wamphamvuyonse, amene anawawitsa moyo wanga,

3 Pakuti moyo wanga wonse ukali mwa ine, Ndi mpweya wa Mulungu m'mphuno mwanga;

4 Milomo yanga siilankhula cosalungama, Ndi lilime langa silichula zacinyengo.

5 Sindibvomereza konse kuti muli olungama; Mpaka kufa ine sinditaya ungwiro wanga.

6 Ndiumirira cilungamo canga, osacileka; Cikhalire moyo ine, mtima wanga sunditonza.

7 Mdani wanga akhale ngati woipa, Ndi iye amene andiukira ngati wosalungama.

8 Pakuti ciyembekezo ca wonyoza Mulungu nciani pomlikhatu Mulungu, Pomcotsera moyo wace?

9 Kodi Mulungu adzamvera kupfuula kwace, ikamdzera nsautso?

10 Kodi adzadzikondweretsa naze Wamphamvuyonse, Ndi kuitana kwa Mulungu nthawi zonse?

11 Ndidzakulangizani za dzanja la Mulungu; Cokhala ndi Wamphamvuyonse sindidzacibisa.

12 Taonani, inu nonse munaciona; Ndipo mugwidwa nazo zopanda pace cifukwa ninji?

13 Ili ndi gawo la munthu woipa kwa Mulungu, Ndi colowa ca akupsinja anzao acilandira kwa Wamphamvtiyonse.

14 Akacuruka ana ace, ndiko kucurukira lupanga, Ndi ana ace sadzakhuta cakudya.

15 Akumtsalira iye adzaikidwa muimfa, Ndi akazi ace amasiye sadzalira maliro.

16 Cinkana akundika ndalama ngati pfumbi, Ndi kukonzeratu zobvala ngati dothi;

17 Azikonzeretu, koma wolungama adzazibvala, Ndi wosalakwa adzagawa ndalamazo.

18 Amanga nyumba yace ngati kadzoce, Ndi ngati wolindira amanga dindiro.

19 Agona pansi ali wacuma, koma saikidwa; Potsegula maso ace, wafa cikomo,

20 Zoopsa zimgwera ngati madzi; Nkuntho umtenga usiku.

21 Mphepo ya kum'mawa Imtenga, nacokaiye; Nimkankha acoke m'malo mwace.

22 Pakuti Mulungu adzamponyera zoopsa, osanlieka; Kuthawa akadathawa m'dzanja lace.

23 Anthu adzamuombera manja, Nadzamuyimbira mluzu acoke m'malo mwace.

28

1 Koma kuli mtapo wa siliva, Ndi malo a golidi amene amuyenga.

2 Citsulo acitenga m'nthaka, Ndi mkuwa ausungunula kumwala.

3 Munthu athawitsa mdima, Nafunafuna mpaka malekezero onse, Miyala ya mdima wa bii ndi ya mthunzi wa imfa.

4 Aboola mgodi posiyana patali pokhala anthu; Aiwalika ndi phazi lopitapo; Apacikika kutali ndi anthu, nalendewa-lendewa.

5 Kunena za nthaka, kucokera momwemo mumaturuka cakudya, Ndi m'munsi mwace musandulizika ngati ndi moto.

6 Miyala yace ndiyo malo a safiro, Ndipo iri nalo pfumbi lagolidi.

7 Njira imeneyi palibe ciombankhanga ciidziwa; Lingakhale diso la kabawi losapenyapo.

8 Nyama zodzikuza sizinapondapo, Ngakhale mkango waukali sunapitapo.

9 Munthu atambasulira dzanja lace kumwala; Agubuduza mapiri kuyambira kumizu.

10 Asema njira pakati pa matanthwe, Ndi diso lace liona ciri conse ca mtengo wace.

11 Atseka mitsinje ingadonthe; Naturutsira poyera cobisikaci.

12 Koma nzeru, idzapezeka kuti? Ndi luntha, malo ace ali kuti?

13 Munthu sadziwa mtengo wace; Ndipo silipezeka m'dziko la amoyo.

14 Pozama pakuti, Mwa ine mulibe; Ndi nyanja ikuti, Kwa ine kulibe.

15 Silipezeka ndi golidi, Sayesapo siliva mtengo wace.

16 Sailinganiza ndi golidi wa Ofiri, Ndi sohamu wa mtengo wace wapatali kapena safiro.

17 Golidi ndi krustalo sizilingana nayo; Ndi kusinthana kwace, siisinthanika ndi zisambiro za golidi woyengetsa.

18 Korali kapena ngale sizikumbukikapo. Mtengo wace wa nzeru uposa wa korali wofiira.

19 Topazi wa Kusi sufanana nayo, Sailinganiza ndi golidi wolongosoka.

20 Koma nzeru ifuma kuti? Ndi luntha, pokhala pace pali kuti?

21 Popeza pabisikira maso a zamoyo zonse, Pabisikiranso mbalame za m'mlengalenga,

22 Cionongeko ndi Imfa zikuti, Tamva mbiri yace m'makutu mwathu.

23 Mulungu ndiye: azindikira njira yace, Ndiye adziwa pokhala pace.

24 Pakuti apenyerera malekezero a dziko lapansi, Naona pansi pa thambo ponse;

25 Pamene anaikira mphepo muyeso wace, Nayesera madzi miyeso;

26 Pakucitira mvula lamulo, Ndi njira yoyendamo mphezi ya bingu;

27 Pamenepo anaiona nzeru, naifotokozera; Anaikonza, naisanthula.

28 Koma kwa munthu anati, Taonani, kuopa Ambuye ndiko nzeru; Ndi kupatukana naco coipa ndiko luntha.

29

1 Ndipo Yobu anaonjezanso mwambi wace, nati,

2 Ha! ndikadakhala monga m'miyezi yapitayi, Monga m'masiku akundisunga Mulungu;

3 Muja nyali yace inawala pamutu panga, Ndipo ndi kuunika kwace ndinayenda mumdima;

4 Monga umo ndinakhala m'masiku anga olimba, Muja uphungu wa Mulungu unakhala pahema panga;

5 Muja Wamphamvuyonse akali nane pamodzi, Ndi ana anga anandizinga;

6 Muja popondera ine padakhatamira ndi mafuta amkaka, Ndi thanthwe linanditsanulira mitsinje ya mafuta aazitona!

7 Muja ndinaturuka kumka kucipata kumudzi, Muja ndinakonza pokhala panga kukhwalala,

8 Anyamata anandiona nabisala, Okalamba anandinyamukira, nakhala ciriri,

9 Akalonga anadziletsa kulankhula, Ndi kugwira pakamwa pao;

10 Mau a omveka anali zi, Ndi lilime lao linamamatira ku malakalaka ao.

11 Pakuti pondimva ine khutu, linandidalitsa; Ndipo pondiona diso, linandicitira umboni.

12 Pakuti ndinapulumutsa wozunzika wakupfuula; Mwana wamasiye yemwe wosowa mthandizi.

13 Dalitso la iye akati atayike linandidzera, Ndi mtima wa mkazi wamasiye ndinauyimbitsa mokondwera.

14 Ndinabvala cilungamo, ndipo cinandibvala ine; Ciweruzo canga cinanga mwinjiro ndi nduwira.

15 Ndinali maso a akhungu, Ndi mapazi a otsimphina.

16 Ndinali atate wa waumphawi; Ndi mlandu wa iye amene sindinamdziwa ndinafunsitsa.

17 Ndipo ndinatyola nsagwada ya wosalungama, Ndi kukwatula cogwidwa kumano kwace.

18 Pamenepo ndinati, Ndidzatsirizika m'cisa canga; Ndipo ndidzacurukitsa masiku anga ngati mcenga.

19 Muzu wanga watambalala kufikira kumadzi; Ndi mame adzakhala pa nthambi yanga usiku wonse.

20 Ulemu wanga udzakhala wosaguga mwa ine, Ndi uta wanga udzakhala wosalifuka m'dzanja mwanga.

21 Anthu anandimvera, nalindira, Nakhala cete, kuti ndiwapangire.

22 Nditanena mau anga sanalankhulanso, Ndi kunena kwanga kunawakhera.

23 Anandilindira ngati kulindira mvula, Nayasama pakamwa pao ngati kulira mvula ya masika.

24 Ndinawaseka akapanda kulimbika mtima; Ndipo sanagwetsa kusangalala kwa nkhope yanga.

25 Ndinawasankhira njira yao ndi kukhala mkuru wao. Ndinakhala ngati mfumu mwa ankhondo ace, Ngati wotonthoza ofedwa.

30

1 Koma tsopano iwo osafikana msinkhu wanga andiseka, Iwo amene atate ao ndikadawapeputsa, osawaika pamodzi ndi agaru olinda nkhosa zanga.

2 Mphamvunso ya m'manja mwao ndikadapindulanji nayo? Ndiwo anthu amene unyamata wao udatha,

3 Atsala mafupa okha okha ndi kusowa ndi njala; Akungudza nthaka youma kuli mdima wa m'cipululu copasuka.

4 Achera terere lokolera kuzitsamba, Ndi cakudya cao ndico mizu ya dinde.

5 Anawapitikitsa pakati pa anthu, Awapfuulira ngati kutsata mbala.

6 Azikhala m'zigwa za cizirezire, M'maenje a m'nthaka ndi m'mapanga.

7 Pakati pa zitsamba alira ngati buru, Pansi pa khwisa asonkhana pamodzi.

8 Ndiwo ana a opusa, inde ana a anthu opanda dzina; Anawaingitsa kuwacotsa m'dziko.

9 Koma tsopano ndasanduka nyimbo ya oterewo, Nandiyesa nthanthi.

10 Anyansidwa nane, akhala patali ndi ine, Saleka kuthira malobvu pankhope panga.

11 Pakuti anamasula nsinga zao, nandizunza; Anataya comangira m'kamwa mwao pamaso panga.

12 Ku dzanja langa lamanja anauka oluluka, Akankha mapazi anga, Andiundira njira zao zakundiononga.

13 Aipsa njira yanga, Athandizana ndi tsoka langa; Ndiwo anthu omwewo osowa mthandizi.

14 Akudza ngati opitira pogamuka linga papakuru, Pakati pa zopasuka adzigubuduza kundidzera ine.

15 Anditembenuzira zondiopsa, Auluza ulemu wanga ngati mphepo; Ndi zosungika zanga zapita ngati mtambo.

16 Ndipo tsopano moyo wanga udzitsanulira m'kati mwanga; Masiku akuzunza andigwira.

17 Nyengo ya usiku mafupa anga awaza mwa ine, Ndi zowawa zondikungudza sizipuma.

18 Mwa mphamvu yaikuru ya nthenda yanga cobvala canga cinasandulika, Cindithina ngati pakhosi pa maraya anga.

19 Iye anandiponya m'matope, Ndipo ndafanana ndi pfumbi ndi phulusa.

20 Ndipfuula kwa Inu, koma simundiyankha; Ndinyamuka, ndipo mungondipenyerera.

21 Mwasandulika kundicitira nkharwe; Ndi mphamvu ya dzanja lanu mundizunza.

22 Mundikweza kumphepo, mundiyendetsa pomwepo; Ndipo mundisungunula mumkuntho.

23 Pakuti ndidziwa kuti mudzandifikitsa kuimfa, Ndi ku nyumba yokomanamo amoyo onse.

24 Koma munthu akati agwe, satambasula dzanja lace kodi? Akati aonongeke, sapfuulako kodi?

25 Kodi sindinamlirira misozi wakulawa zowawa? Kodi moyo wanga sunacitira cisoni osowa?

26 Muja ndinayembekeza cokoma cinadza coipa, Ndipo polindira kuunika unadza mdima.

27 M'kati mwanga mupweteka mosapuma, Masiku a mazunzo andidzera.

28 Ndiyenda ndiri wothimbirira osati ndi dzuwa ai; Ndinyamuka mumsonkhano ndi kupfuula,

29 Ndiri mbale wao wa ankhandwe, Ndi mnansi wao wa nthiwatiwa.

30 Khungu langa lada, nilindipfundukira; Ndi mafupa anga awawa ndi kutentha kwao.

31 Cifukwa cace zeze wanga wasandulika wa maliro, Ndi citoliro canga ca mau a olira misozi.

31

1 Ndinapangana ndi maso anga, Potero ndipenyerenji namwali?

2 Pakuti gawo la Mulungu locokera kumwamba, Ndi colowa ca Wamphamvuyonse cocokera m'mwambamo nciani?

3 Si ndizo cionongeko ca wosalungama, Ndi tsoka la ocita mphulupulu?

4 Nanga sapenyanjira zanga, Ndi kuwerenga moponda mwanga monse?

5 Ngati ndinayanjana nalo bodza, Ndi phazi langa linathamangira cinyengo;

6 Andiyese ndi muyeso wolingana, Kuti Mulungu adziwe ungwiro wanga.

7 Ngati phazi langa linapambuka m'njira, Ndi mtima wanga unatsata maso anga? Ngati cirema camamatira manja anga?

8 Ndibzale ine nadye wina, Ndi zondimerera ine zizulidwe.

9 Ngati mtima wanga wakopeka ndi mkazi, Ngati ndalalira pa khomo la mnzanga,

10 Mkazi wanga aperere wina; Wina namuike kumbuyo.

11 Pakuti ico ndi coipitsitsa, Ndico mphulupulu yoyenera oweruza anene mlandu wace.

12 Pakuti ndico moto wakunyeka mpaka cionongeko, Ndi cakuzula zipatso zanga zonse.

13 Ngati ndapeputsa mlandu wa kapolo wanga, kapena wa mdzakazi wanga, Potsutsana nane iwo,

14 Ndidzatani ponyamuka Mulungu? Ndipo pondizonda Iye ndidzamyankha ciani?

15 Kodi Iye amene anandilenga ine m'mimba sanamlenga iyenso? Sindiye mmodzi anatiumba m'mimba?

16 Ngati ndakaniza aumphawi cifuniro cao, Kapena kutopetsa maso a amasiye,

17 Kapena kudya nthongo yanga ndekha, Osadyako mwana wamasiye;

18 (Pakuti kuyambira ubwana wanga analeredwa ndi ine monga ndi atate; Ndipo ndinakhala nkhoswe ya wamasiye cibadwire ine.)

19 Ngati ndinaona wina alinkutayika wopanda cobvala, Kapena kuti wosowa alibe copfunda;

20 Ngati zuuno zace sizinandiyamika, Ngati sanapfunda ubweya wa nkhosa zanga;

21 Ngati ndinasamulira ana amasiye dzanja langa, Popeza ndinaona thandizo langa kucipata;

22 Libanthuke phewa langa paphalo, Ndi dzanja langa liduke pagwangwa.

23 Pakuti tsoka locokera kwa Mulungu linandiopsa, Ndi cifukwa ca ukulu wace sindinakhoza kanthu,

24 Ngati ndayesa golidi ciyembekezo canga, Ndi kunena ndi golidi woyengetsa, Ndiwe cikhazikitso canga;

25 Ngati ndinakondwera popeza cuma canga ncacikuru, Ndi dzanja langa lapeza zocuruka;

26 Ngati ndalambira dzuwa lirikuwala, Kapena mwezi ulikuyenda monyezimira;

27 Ndi mtima wanga wakopeka m'tseri, Ndi pakamwa panga padapsompsona dzanja langa;

28 Icinso ndi mphulupulu yoyenera oweruza kunena mlandu wace; Pakuti ndikadakana Mulungu ali m'mwamba.

29 Ngati ndakondwera nalo tsoka la wondida, Kapena kudzitukula pompeza coipa;

30 Ndithu sindinalola m'kamwa mwanga mucimwe, Kupempha motemberera moyo wace.

31 Ngati amuna a m'hema mwanga sanati, Ndani adzapeza munthu wosakhuta nyama yomgawira Yobu?

32 Mlendo sakagona pakhwalala, Koma ndinatsegulira wam'njira pakhomo panga.

33 Ngati ndakwirira zolakwa zanga monga Adamu, Ndi kubisa mphulupulu yanga m'cifuwa mwanga;

34 Popeza ndinaopa unyinji waukuru, Ndi cipepulo ca mapfuko cinandiopsetsa; Potero ndinakhala cete osaturuka pakhomo panga.

35 Ha! ndikadakhala naye wina wakundimvera, Cizindikilo canga sici, Wamphamvuyonse andiyankhe; Mwenzi ntakhala nao mau akundineneza analemberawo mdani wangal

36 Ndithu ndikadawasenza paphewa panga, Ndi kudzimangirira awa ngati korona.

37 Ndikadamfotokozera ciwerengo ca mopondamo mwanga, Ndikadamsenderera Iye ngati ka longa,

38 Ngati minda yanga ipfuula monditsutsa, Ndi nthumbira zace zilira pamodzi;

39 Ngati ndadya zipatso zace wopanda ndarama, Kapena kutayitsa eni ace moyo wao;

40 Imere minga m'malo mwa tirigu, Ndi dawi m'malo mwa barele. Mau a Yobu atha.

32

1 Pamenepo amuna atatuwa analeka kumyankha Yobu; pakuti anali wolungama pamaso pace pa iye mwini.

2 Ndipo adapsa mtima Elihu mwana wa Barakeli wa ku Buzi, wa cibale ca Ramu, adapsa mtima pa Yobu; pakuti anadziyesera yekha wolungama, wosati Mulungu.

3 Adapsa mtima pa mabwenzi ace atatu omwe, pakuti anasowa pomyankha; koma anamtsutsa Yobu kuti ali woipa.

4 Ndipo Elihu analindira kulankhula ndi Yobu, popeza akulu misinkhu ndi iwowa.

5 Koma pakuona Elihu kuti anthu atatuwa anasowa poyankha pakamwa pao anapsa mtima.

6 Ndipo Elihu mwana wa Barakeli wa ku Buzi anayankha, nati, Ine ndine mnyamata, inu ndinu okalamba; Cifukwa cace ndinadziletsa, ndi kuopa kukuonetsani monga umo ndayesera ine.

7 Ndinati, Amisinkhu anene, Ndi a zaka zocuruka alangize nzeru.

8 Koma m'munthu muli mzimu, Ndi mpweya wa Wamphamvuyonse wawazindikiritsa.

9 Akulu sindiwo eni nzeru, Ndi okalamba sindiwo ozindikira ciweruzo.

10 Cifukwa cace ndinati, Ndimvereni ine, Inenso ndidzaonetsa monga umo ndayesera ine.

11 Taonani, ndinalindira mau anu, Ndinacherera khutu zifukwa zanu, Pofunafuna inu ponena.

12 Inde ndinasamalira inu; Koma taonani, panalibe womtsutsa Yobu, Kapena wakumbwezera mau pakati painu.

13 Msamati, Tapeza nzeru ndife, Mulungu akhoza kumkhulula, si munthu ai;

14 Popeza sanandiponyera ine mau, Sindidzamyankha ndi maneno anu.

15 Asumwa, sayankhanso, Anawathera mau.

16 Kodi ndidzangolindira popeza sanena iwo, Popeza akhala du osayankhanso?

17 Ndidzayankha inenso mau anga, Ndidzaonetsa inenso za m'mtima mwanga.

18 Pakuti ndadzazidwa ndi mau, Ndi mzimu wa m'kati mwanga undifulumiza.

19 Taonani, m'cifuwa mwanga muli ngati vinyo wosowa popungulira, Ngati matumba atsopano akuti aphulike.

20 Ndidzanena kuti cifundo citsike; Ndidzatsegula milomo yanga ndi kuyankha.

21 Ndisati ndisamalire nkhope ya munthu, Kapena kumchula munthu maina omdyola nao;

22 Pakuti sindidziwa kuchula maina osyasyalika; Ndikatero Mlengi wanga adzandicotsa msanga.

33

1 Komatu, Yobu, mumvere maneno anga, Mucherere khutu mau anga.

2 Taonani tsono, ndatsegula pakamwa panga, Lilime langa lanena m'kamwa mwanga.

3 Maneno anga aulula ciongoko ca mtima wanga, Ndi monga umo idziwira milomo yanga idzanena zoona.

4 Mzimu wa Mulungu unandilenga, Ndi mpweya wa Wamphamvuyonse umandipatsa moyo.

5 Ngati mukhoza, mundiyankhe; Mulongosolere mau anu pamaso panga, mukonzeke.

6 Taonani, ndikhala kwa Mulungu ngati inu; Inenso ndinaumbidwa ndi dothi,

7 Taonani, kuopsa kwanga simudzacita nako mantha; Ndi ici ndikusenzetsani sicidzakulemererani.

8 Zedi mwanena m'makutu mwanga, Ndinamvanso mau akunena kwanu, akuti,

9 Ndine woyera ine, wopanda kulakwa, Ndine wosaparamula, ndiribe mphulupulu.

10 Taonani, Iye apeza zifukwa zoti anditsutse nazo, Andiyesa mdani wace;

11 Amanga mapazi anga m'zigologolo, Ayang'anira poyenda ine ponse.

12 Taonani, ndidzakuyankhani m'mene muli mosalungama; Pakuti Mulungu ndiye wamkulu woposa munthu.

13 Mutsutsana ndi Iye cifukwa ninji? Popeza pa zace zonse saulula cifukwa.

14 Pakuti Mulungu alankhula kamodzi, Kapena kawiri, koma anthu sasamalira.

15 M'kulota, m'masomphenya a usiku, Pakuwagwera anthu tulo tatikuru, Pogona mwacheru pakama,

16 Pamenepo atsegula makutu a anthu, Nakomera cizindikilo cilangizo cao;

17 Kuti acotse munthu ku cimene akadacita, Ndi kubisira munthu kudzikuza kwace;

18 Kuti amletse angaonongeke, Ndi moyo wace ungatayike ndi lupanga.

19 Alangidwanso ndi zowawa pakama pace, Ndi kulimbana kowawa kosapuma m'mafupa ace.

20 M'mwemo mtima wace ucita mseru ndi mkate, Ndi moyo wace pa cakudya colongosoka.

21 Mnofu wace udatha, kuti sungapenyeke; Ndi mafupa ace akusaoneka aturuka.

22 Inde wasendera kufupi ku manda, Ndi moyo wace kwa akuononga.

23 Akakhala kwa iye mthenga, Womasulira mau mmodzi mwa cikwi, Kuonetsera munthu comuyenera;

24 Pamenepo Mulungu amcitira cifundo, nati, Mlanditse, angatsikire kumanda, Ndampezera dipo.

25 Mnofu wace udzakhala se, woposa wa mwana; Adzabwerera ku masiku a ubwana wace.

26 Apembedza Mulungu, ndipo amkomera mtima; M'mwemo aona nkhope yace mokondwera; Ndipo ambwezera munthu cilungamo cace.

27 Apenyerera anthu, ndi kuti, Ndinacimwa, ndaipsa coongokaco, Ndipo sindinapindula nako.

28 Koma anandiombola ndingatsikire kumanda, Ndi moyo wanga udzaona kuunika.

29 Taona, izi zonse azicita Mulungu Kawiri katatu ndi munthu,

30 Kumbweza angalowe kumanda, Kuti kuunika kwa moyo kumuwalire.

31 Cherani khutu, Yobu, mundimvere ine; Mukhale cete, ndipo ndidzanena ine.

32 Ngati muli nao mau mundiyankhe. Nenani, pakuti ndifuna kukulungamitsani.

33 Ngati mulibe mau, tamverani Ine; Mukhale cete, ndipo ndizakuphunzitsani nzeru.

34

1 Ndipo Elihu anabwereza kunena, nati,

2 Tamverani mau anga, inu anzeru; Mundicherere khutu inu akudziwa.

3 Pakuti khutu liyesa mau, Monga m'kamwa mulawa cakudya.

4 Tidzisankhire coyeneraco, Tidziwe mwa tokha cokomaco.

5 Pakuti Yobu wanena, Ine ndine wolungama, Ndipo Mulungu wandicotsera coyenera ine.

6 Kodi ndidzinamizire? Bala langa nlosapola, ngakhale sindinalakwa.

7 Wakunga Yobu ndani, Wakumwa mwano ngati madzi?

8 Wakutsagana nao ocita mphulupulu, Nayendayenda nao anthu oipa.

9 Pakuti anati, Munthu sapindula kanthu nako Kubvomerezana naye Mulu ngu.

10 Cifukwa cace mundimvere ine, eni nzeru inu, Nkutali ndi Mulungu kucita coipa, Ndi Wamphamvuyonse kucita cosalungama.

11 Pakuti ambwezera munthu monga mwa nchito yace, Napezetsa munthu ali yense monga mwa mayendedwe ace.

12 Ndithu zoonadi, Mulungu sangacite coipa, Ndi Wamphamvuyonse sangaipse mlandu.

13 Anamuikiza dziko lapansi ndani? Kapena anakonzeratu dziko lonse lokhalamo anthu ndani?

14 Akadzikumbukila yekha mumtima mwace, Akadzisonkhanitsira yekha mzimu wace ndi mpweya wace,

15 Zamoyo zonse zidzatsirizika pamodzi, Ndi munthu adzabwerera kupfumbi.

16 Ngati tsono uli nako kuzindikira, tamvera ici, Cherera khutu kunena kwanga.

17 Kodi munthu woipidwa naco ciweruzo adzalamulira? Ndipo kodi utsutsa wolungama ndi wamphamvuyo kuti ngwoipa?

18 Kodi kuyenera kunena kwa mfumu, Wopanda pace iwe, Kapena kwa akalonga, Oipa inu?

19 Nanga kwa Iye wosasamalira nkhope za akalonga, Wosasiyanitsa pakati pa wolemera ndi wosauka? Pakuti onsewo ndiwo nchito ya manja ace.

20 M'kamphindi akufa, ngakhale pakati pa usiku, Anthu agwedezeka, napita, Amphamvu acotsedwa opanda dzanja lakuwacotsa.

21 Pakuti maso ace ali pa njira ya munthu ali yense, Napenya moponda mwace monse.

22 Palibe mdima kapena mthunzi wa imfa, Kuti ocita zopanda pace abisaleko.

23 Pakuti Mulungu alibe cifukwa ca kulingiriranso za munthu, Kuti afike kwa. Iye kudzaweruzidwa.

24 Aphwanya eni mphamvu osaturutsa kubwalo mlandu wao, Naika ena m'malo mwao.

25 Pakuti asamalira nchito zao, Nawagubuduza usiku kuti aphwanyike.

26 Awakantha ngati oipa, Poyera pamaso pa anthu.

27 Popeza anapambuka, naleka kumtsata, Osasamalira njira zace ziri zonse.

28 M'mwemo anafikitsa kwa Iye kupfuula kwa osauka; Ndipo anamva Iye kupfuula kwa ozunzika.

29 Iye akapatsa mpumulo adzamtsutsa ndani? Akabisa nkhope yace adzampenyerera ndani? Cikacitika pa mtundu wa anthu, kapena pa munthu, ncimodzimodzi;

30 Kuti munthu wonyoza Mulungu asacite ufumu, Ndi anthu asakodwe mumsampha,

31 Pakuti pali wina kodi anati kwa Mulungu, Ndasenza kulanga kwanu, ndingakhale sindinalakwa?

32 Cimene sindiciona mundilangize ndi Inu, Ngati ndacita cosalungama sindidzabwerezanso.

33 Kodi cilango ca Mulungu cikhale monga mucifuna inu, pakuti mucikana? Musankhe ndi inu, ine ai; M'mwemo monga mudziwa, nenani.

34 Anthu ozindikira adzanena nane, Inde anthu anzeru onse akundimva adzati,

35 Yobu alankhula wopanda kudziwa, Ndi mau ace alibe nzeru.

36 Mwenzi nayesedwe Yobu kufikira kutha, Cifukwa ca kuyankha kwace monga anthu amphulupulu,

37 Pakuti pa kucimwa kwace aonjeza kupikisana ndi Mulungu, Asansa manja pakati pa ife, Nacurukitsa maneno ace pa Mulungu.

35

1 Ndipo Elihu anabwereza kunena, nati,

2 Kodi muciyesa coyenera, Umo mukuti, Cilungamo canga ciposa ca Mulungu,

3 Pakuti munena, Upindulanji naco? Posacimwa ndinapindula ciani cimene sindikadapindula pocimwa?

4 Ndidzakuyankhani, Ndi anzanu pamodzi ndi inu.

5 Yang'anani kumwamba, nimuone, Tapenyani mitambo yokwera yakuposa inu.

6 Ngati mwacimwa, mumcitira Iye ciani? Zikacuruka zolakwa zanu, mumcitira Iye ciani?

7 Mukakhala wolungama, mumninkhapo ciani? Kapena alandira ciani pa dzanja lanu?

8 Coipa canu cikhoza kuipira munthu wonga inu, Ndi cilungamo canu cikhoza kukomera wobadwa ndi munthu.

9 Cifukwa ca kucuruka masautso anthu anapfuula, Apfuula cifukwa ca dzanja la amphamvu.

10 Koma palibe anganene, Ali kuti Mulungu Mlengi wanga, Wakupatsa nyimbo usiku;

11 Wakutilangiza ife koposa nyama za padziko, Wakutipatsa nzeru zoposa mbalame za m'mlengalenga?

12 Apo apfuula, koma Iye sawayankha; Cifukwa ca kudzikuza kwa anthu oipa.

13 Zedi Mulungu samvera zacabe, Ndi Wamphamvuyonse sazisamalira.

14 Inde mungakhale munena, Sindimpenya, Mlanduwo uli pamaso pace, ndipo mumlindira.

15 Ndipo tsopano popeza analibe kumzonda m'kukwiya kwace, Ndi kusamalitsa colakwa,

16 Cifukwa cace Yobu anatsegula pakamwa pace mwacabe, Nacurukitsa mau opanda nzeru.

36

1 Elihu nabwereza, nati,

2 Mundilole pang'ono, ndidzakuuzani, Pakuti ndiri naonso mau akunenera Mulungu.

3 Ndidzatenga nzeru zanga kutali, Ndidzabvomereza kuti Mlengi wanga ndi wolungama.

4 Pakuti zoonadi, mau anga sali abodza, Wakudziwitsa mwangwiro ali nanu.

5 Taonani, Mulungu ndiye mwini mphamvu, ndipo sapeputsa munthu; Mphamvu ya nzeru zace ndi yaikuru.

6 Sasunga woipa akhale ndi moyo, Koma awaninkha ozunzikazowayenera iwo.

7 Sawacotsera wolungama maso ace, Koma pamodzi ndi mafumu pa mpando wao Awakhazika cikhazikire, ndipo akwezeka.

8 Ndipo akamangidwa m'nsinga, Nakakodwa ndi zingwe za mazunzo,

9 Pamenepo awafotokozera nchito zao, Ndi zolakwa zao, kuti anacita modzikuza.

10 Awatseguliranso m'khutu mwao kuti awalangize, Nawauza abwerere kuleka mphulupulu.

11 Akamvera ndi kumtumikira, Adzatsiriza masiku ao modala, Ndi zaka zao mokondwera.

12 Koma akapanda kumvera adzatayika ndi lupanga, Nadzatsirizika osadziwa kanthu.

13 Koma iwo a mtima wakunyoza Mulungu, akundika mkwiyo, Akawamanga Iye, sapfuulira.

14 Iwowa akufa akali biriwiri, Ndi moyo wao utayika ngati odetsedwa.

15 Apulumutsa wozunzika mwa kuzunzika kwace, Nawatsegulira m'khutu mwao mwa kupsinjika kwao.

16 Inde akadakukopani mucoke posaukira, Mulowe kucitando kopanda copsinja; Ndipo zoikidwa pagome panu zikadakhala zonona ndithu.

17 Koma mukadzazidwa nazo zolingirira oipa, Zolingirirazo ndi ciweruzo zidzakugwiranibe,

18 Pakuti mucenjere, mkwiyo ungakunyengeni mucite mnyozo; Ndipo usakusokeretseni ukulu wa dipoli.

19 Cuma canu cidzafikira kodi, kuti simudzakhala wopsinjika, Kapena mphamvu yanu yonse yolimba?

20 Musakhumbe usiku, Umene anthu alikhidwe m'malo mwao.

21 Cenjerani, musaluniike kumphulupulu; Pakuti mwaisankha iyi mutazunzidwa.

22 Taonani, Mulungu acita mokwezeka mu mphamvu yace, Mphunzitsi wakunga Iye ndani?

23 Anamuikira njira yace ndani? Adzati ndani, Mwacita cosalungama?

24 Kumbukilani kuti mukuze nchito zace, Zimene anaziyimbira anthu.

25 Anthu onse azipenyerera, Anthu aziyang'anira kutali.

26 Taonani, Mulungu ndiye wamkuru, ndipo sitimdziwa; Ciwerengo ca zaka zace ncosasanthulika.

27 Pakuti akweza madontho a mvula, Akhetsa mvula ya m'nkhungu yace

28 Imene mitambo itsanulira, Nibvumbitsira anthu mocuruka.

29 Pali munthu kodi wodziwitsa mayalidwe a mitambo, Ndi kugunda kwa msasa wace?

30 Taonani, Iye ayala kuunika kwace pamenepo. Nabvundikira kunsi kwace kwa nyanja.

31 Pakuti aweruza nazo mitundu ya anthu. Apatsa cakudya cocuruka.

32 Akutidwa manja ace ndi mphezi, Nailamulira igwere pofunapo Iye.

33 Kugunda kwace kulalikira za Iye, Zoweta zomwe zilota mtambo woyandikira.

37

1 Pa icinso mtima wanga unienjemera, Nusunthika m'malo mwace.

2 Mvetsetsani cibumo ca mau ace, Ndi kugunda koturuka m'kamwa mwace.

3 Akumveketsa pansi pa thambo ponse, Nang'anipitsa mphezi yace ku malekezero a dziko lapansi.

4 Mau abuma kuitsata, Agunda ndi mau a ukulu wace, Ndipo sailetsa atamveka mau ace,

5 Mulungu agunda modabwitsa ndi mau ace, Acita zazikuru osazidziwa ife.

6 Pakuti anena kwa cipale cofewa, Ugwe padziko. Momwemonso kwa mvula, Ndi kwa mbvumbi waukuru.

7 Atsekereza mokhomera cizindikilo dzanja la munthu ali yense, Kuti anthu onse anawalenga adziwe.

8 Pamenepo zirombo zilowa mobisalamo, Nizikhala m'ngaka mwao.

9 M'cipinda mwace muturuka kabvumvulu, Ndi cisanu cifuma kumpoto.

10 Mwa kupuma kwace apereka cipale, Ndi madzi acitando aundana.

11 Asenzetsanso mtambo wakuda bii madzi, Afunyulula mtambo wokhalamo mphezi yace;

12 Ndipo utembenuka-tembenuka pakulangiza kwace, Kuti ucite ziri zonse aulamulira, Pa nkhope ya dziko lokhalamo anthu;

13 Ngati aufikitsira dziko lace kulidzudzula, Kapena kulicitira cifundo.

14 Tamverani ici, Yobu. Taimani, mulingirire zodabwiza za Mulungu.

15 Kodi mudziwa umo Mulungu azilangizira zimenezi, Nawalitsa mphezi ya m'mtambo mwace?

16 Kodi mudziwa madendekeredwe ace a mitambo, Zodabwiza za Iye wakudziwa mwangwiro?

17 Kodi mudziwa umo zobvala zanu zifundira, Pamene dziko liri thuu cifukwa ca mwela?

18 Kodi muyala thambo pamodzi ndi Iye, Ndilo lolimba ngati kalirole woyengeka?

19 Mutilangize cimene tidzanena ndi Iye; Sitidziwa kulongosola mau athu cifukwa ca mdima.

20 Kodi munthu ayenera kumuuza kuti ndifuna kunena, Kapena kodi munthu adzakhumba kumezedwa?

21 Ndipo tsopano anthu sakhoza kupenyerera kuunika pakunyezimira kuthambo, Ndi mphepo yapita ndi kuuyeretsa,

22 Kucokera kumpoto kudzera kuwala konyezimira, Mulungu ali nao ukulu woopsa.

23 Kunena za Wamphamvuyonse, sitingamsanthule; ndiye wa mphamvu yoposa; Koma mwa ciweruzo ndi cilungamo cocuruka samasautsa.

24 M'mwemo anthu amuopa, Iye sasamalira ali yense wanzeru mumtima.

38

1 Pamenepo Yehova anayankha Yobu m'kabvumvulu, nati,

2 Ndani uyu adetsa uphungu, Ndi mau opanda nzeru?

3 Udzimangire m'cuuno tsono ngati mwamuna; Ndikufunsa, undidziwitse.

4 Unali kuti muja ndinaika maziko a dziko lapansi? Fotokoza ngati udziwa kuzindikira.

5 Analemba malire ace ndani, papeza udziwa? Anayesapo cingwe cace ndani?

6 Maziko ace anakumbidwa pa ciani? Kapena anaika ndani mwala wace wa pangondya,

7 Muja nyenyezi za m'mawa zinayimba limodzi mokondwera, Ndi ana onse a Mulungu anapfuula ndi cimwemwe?

8 Kapena anatseka nyanja ndani ndi zitseko, Muja idakamula ngati kuturuka m'mimba,

9 Muja ndinayesa mtambo cobvala cace, Ndi mdima wa bii nsaru yace yakulunga,

10 Ndi kuilembera malire anga, Ndi kuika mipikizo ndi zitseko,

11 Ndi kuti, Ufike mpaka apa, osapitirirapo; Apa adzaletseka mafunde ako odzikuza?

12 Kodi walamulira m'mawa ciyambire masiku ako, Ndi kudziwitsa mbanda kuca malo ace;

13 Kuti agwire malekezero a dziko lapansi, Nakutumule oipa acokeko?

14 Lisandulika ngati dothi lonyata pansi pa cosindikiza, Ndi zonse zibuka ngati cobvala;

15 Ndi kuunika kwa oipa kuletsedwa kuti asakuone, Ndi dzanja losamulidwa lityoledwa.

16 Kodi unalowa magwero a nyanja? Kodi unayendayenda pozama peni peni?

17 Kodi zipata za imfa zinabvumbulukira iwe? Kapena kodi unaona zipata za mthunzi wa imfa?

18 Kodi unazindikira citando ca dziko lapansi? Fotokozera, ngati ucidziwa conse.

19 Iri kuti njira yomukira pokhala kuunika? Ndi mdima, pokhala pace pali kuti,

20 Kuti upite nao ku malire ace, Kuti uzindikire miseu ya ku nyumba yace?

21 Udziwa, pakuti unabadwa pamenepo, Ndi masiku ako acuruka kuwerenga kwao.

22 Kodi unalowa m'zosungiramo cipale cofewa? Kapena unapenya zosungiramo matalala,

23 Amene ndiwasungira tsiku la nsautso, Tsiku lakulimbana nkhondo?

24 Njira iri kuti yomukira pogawikana kuunika, Kapena pomwazikira mphepo ya kum'mawa pa dziko lapansi?

25 Ndani anacikumbira mcera cimvula, Kapena njira ya bingu la mphezi,

26 Kubvumbitsa mvula pa dziko lapanda anthu, Ku cipululu kosakhala munthu,

27 Kukhutitsa thengo la kunkhwangwala, Ndi kuphukitsa msipu?

28 Kodi mvula iri naye atate? Kapena wabala ndani madontho amame?

29 Cipale cinaturuka m'inimba ya yani? Ndi cisanu cocokera m'mwamba anacibala ndani?

30 Madzi aundana ngati mwala, Ndi pamwamba pa nyanja yozama mpogwirana madzi.

31 Kodi ungamange gulu la Nsangwe? Kapena kumasula zomangira za Akamwiniatsatana?

32 Ungaturutse kodi nyenyezi m'nyengo zao monga mwa malongosoledwe ao? Kapena kutsogolera Mlalang'amba ndi ana ace?

33 Kodi udziwa malemba a kuthambo? Ukhoza kukhazikitsa ufumu wao pa dziko lapansi?

34 Kodi udziwa kukwezera mau ako kumitambo, Kuti madzi ocuruka akukute?

35 Kodi ukhoza kutumiza mphezi kuti zimuke, Ndi kunena nawe, Tiri pano?

36 Ndani analonga nzeru m'mitambomo? Ndani waninkha nyenyezi yotsotsoka luntha?

37 Adziwa ndani kuwerenga mitambo mwanzeru, Ndi kutsanulira micenje ya kuthambo ndani,

38 Pokandika pfumbi, Ndi kuundana zibuma pamodzi?

39 Kodi ukhoza kusakira mkango waukazi nyama? Ndi kukwaniritsa cakudya ca misona,

40 Pamene ibwathama m'ngaka mwao, Nikhala mobisala kulaliramo?

41 Amkonzeratu khungubwi cakudya cace ndani, Pamene ana ace apfuulira kwa Mulungu, Nauluka-uluka osowa cakudya?

39

1 Kodi udziwa nyengo yakuswana zinkhoma? Kodi wapenyerera pakuswa nswala?

2 Ukhoza kodi kuwerenga miyezi yakuzipitira, Kapena udziwa nyengo yoti ziswane?

3 Zithuntha, ziswa, Zitaya zowawa zao.

4 Ana ao akhala ojinca, akulira kuthengo, Acoka osabwerera kwa amao.

5 Ndani walola mbidzi ituruke yaufulu? Anaimasulira mbidzi nsinga zace ndani,

6 Imene ndaciyesa cipululu nyumba yace, Ndi dziko lakhulo pokhala pace?

7 Aseka phokoso la kumudzi, Osamva kukuwa kwa wofulumiza nyama za m'goli.

8 Poyenda ponse pamapiri mpa busa pace; Ilondola caciwisi ciri conse.

9 Kodi njati idzabvomera kukutumikira, Idzakhala ku codyetseramo cako kodi?

10 Kodi ukhoza kumanga njati ndi lamba lace ilime m'mcera? Kapena idzakutsata kodi kufafaniza nthumbira m'zigwa?

11 Udzaikhulupirira kodi, popeza mphamvu yace njaikuru? Udzaisiyira nchito yako kodi?

12 Kodi udzaitama kuti itute mbeu zako, Ndi kuzisonkhanitsira kudwale?

13 Phiko la nthiwatiwa likondwera, Koma mapiko ndi nthenga zace nzofatsa kodi?

14 Pakuti isiya mazira ace panthaka, Nimafunditsa m'pfumbi,

15 Niiwala kuti phazi lingawaphwanye, Kapena cirombo cingawapondereze.

16 Iumira mtima ana ace monga ngati sali ace; Idzilemetsa ndi nchito cabe, popeza iribe mantha;

17 Pakuti Mulungu anaimana nzeru, Ndipo sanaigawira luntha.

18 Ikafika nthawi yace, iweramuka, Iseka kavalo ndi wa pamsana pace.

19 Wampatsa kavalo mphamvu yace kodi? Wambveka pakhosi pace cenjerere cogwedezeka?

20 Wamlumphitsa kodi ngati dzombe? Ulemerero wa kumina kwace ngwoopsa.

21 Apalasa kucigwa, nakondwera nayo mphamvu yace; Aturuka kukomana nao eni zida.

22 Aseka mantha osaopsedwa, Osabwerera kuthawa lupanga.

23 Phodo likuti koco koco panthiti pace, Mkondo wonyezimira ndi nthungo yomwe.

24 Ndi kunjenjemera kwaukali aimeza nthaka, Osaimitsika pomveka lipenga.

25 Pomveka lipenga akuti, Hee! Anunkhiza nkhondo irikudza kutali Kugunda kwa akazembe ndi kuhahaza,

26 Kodi kabawi auluka mwa nzeru zako, Natambasula mapiko ace kumka kumwera?

27 Kodi ciombankhanga cikwera m'mwamba pocilamulira iwe, Nicimanga cisanja cace m'mwamba?

28 Kwao nku thanthwe, cigona komweko, Pansonga pa thanthwe pokhazikikapo.

29 Pokhala kumeneko ciyang'ana cakudya; Maso ace acipenyetsetsa ciri kutali,

30 Ana ace akumwa mwazi, Ndipo pomwe pali ophedwa, apo pali ico.

40

1 Ndipo Yehova anabwereza kwa Yobu, nati,

2 Kodi wodzudzulayo atsutsane ndi Wamphamvuyonse? Wocita makani ndi Mulungu ayankhe.

3 Pamenepo Yobu anayankha Yehova, nati,

4 Taonani, ndakhululuka ine, ndidzakubwezerani mau otani? Ndigwira pakamwa.

5 Ndalankhula kamodzi, koma sindidzayankha; Inde kawiri, koma sindionjezanso.

6 Ndipo Yehova anamyankha Yobu m'kabvumvulu, nati,

7 Dzimangire m'cuuno tsono ngati mwamuna; Ndidzakufunsa, undidziwitse.

8 Cingakhale ciweruzo canga udzacityola kodi? Udzanditsutsa kuti ndiri woipa kodi, kuti ukhale wolungama ndiwe?

9 Kodi uli nalo dzanja ngati Ine Mulungu? Kapena ukhoza kugunda ndi mau ngati Ine?

10 Udzikometsere tsono ndi ukulu ndi kukuzika, Nubvale ulemu ndi ulemerero.

11 Tsanulira mkwiyo wako wosefuka, Nupenyerere ali yense wodzikuza ndi kumcepetsa,

12 Upenyerere ali yense wodzikuza, numtsitse, Nupondereze oipa pomwe akhala.

13 Uwakwirire pamodzi m'pfumbi, Uzimange nkhope zao pobisika.

14 Pamenepo inenso ndidzakubvomereza, Kuti dzanja lako lako lamanja likupulumutsa.

15 Tapenya tsono mvuu ndinaipanga pamodzi ndi iwe, Ikudya udzu ngati ng'ombe.

16 Tapenya tsono, mphamvu yace iri m'cuuno mwace, Ndi kulimbalimba kwace kuli m'mitsempha ya m'mimba yace.

17 Igwedeza mcira wace ngati mkungudza; Mitsempha ya ncafu zace ipotana.

18 Mafupa ace akunga misiwe yamkuwa; Ziwalo zace zikunga zitsulo zamphumphu,

19 Iyo ndiyo ciyambi ca macitidwe a Mulungu; Wakuilenga anaininkha lupanga lace.

20 Pakuti mapiri aiphukitsira cakudya, Kumene zisewera nyama zonse za kuthengo,

21 Igona pansi patsinde pa mitengo yamthunzi, Pobisala pabango ndi pathawale.

22 Mitengo yamthunzi iiphimba ndi mthunzi wao, Misondodzi ya kumtsinje iizinga.

23 Taona madzi a mumtsinje akakula, siinjenjemera; Ilimbika mtima, ngakhale Yordano atupa mpaka pakamwa pace,

24 Ikakhala maso, munthu adzaigwira kodi? Kapena kuboola m'mphuno mwace iri m'khwekhwe?

41

1 Kodi ukhoza kukoka ng'ona ndi mbedza? Kapena kukanikiza kalandira wace ndi cingwe?

2 Kodi ukhoza kumanga m'mphuno ndi mlulu? Kapena kuboola nsagwada wace ndi momba?

3 Kodi idzacurukitsa mau akukupembedza? Kapena idzanena nawe mau ofatsa?

4 Kodi idzapangana ndi iwe, Kuti uitenge ikhale kapolo wako wacikhalire?

5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame? Kapena udzaimangira anamwali ako kuti aiwete?

6 Kodi opangana malonda adzaitsatsa? Adzaigawana eni malonda?

7 Kodi udzadzaza khungu lace ndi nchetho, Kapena mutu wace ndi miomba?

8 Isanjike dzanja lako; Ukakumbukila nkhondoyi, sudzateronso.

9 Taona, ciyembekezo cako ca pa iyo cipita pacabe. Kodi sadzatenga nkhawa munthu pakungoiona?

10 Palibe wolimba mtima kuti adzaiputa. Ndipo ndaniyo adzaima pamaso pa Ine?

11 Ndaniyo anayamba kundipatsa Ine kuti ndimthokoze? Ziri zonse pansi pa thambo ponse ndi zanga.

12 Sindikhala cete osachula ziwalo za ng'onayo, Ndi mbiri ya mphamvu yace, ndi makonzedwe ace okoma.

13 Ndani adzasenda cobvala cace cakunja? Adzalowa ndani ku mizere iwiri ya mano ace?

14 Adzatsegula ndani zitseko za pakamwa pace? Mano ace aopsa pozungulira pao.

15 Maamba ace olimba ndiwo kudzitama kwace; Amangika pamodzi ngati okomeredwatu.

16 Alumikizana lina ndi linzace, Mphepo yosalowa pakati pao.

17 Amamatirana lina ndi linzace, Agwirana osagawanikana.

18 Pakuyetsemula ing'anipitsa kuunika, Ndi maso ace akunga zikope za m'mawa.

19 M'kamwa mwace muturuka miuni, Mbaliwali za moto zibukamo.

20 M'mphuno mwace muturuka utsi, Ngati nkhali yobwadamuka ndi moto wa zinyatsi.

21 Mpweya wace uyatsa makara, Ndi m'kamwa mwace muturuka lawi la moto.

22 Kukhosi kwace kukhala mphamvu, Ndi mantha abvumbuluka patsogolo pace,

23 Nyama yace yopsapsala igwirana Ikwima pathupi pace yosagwedezeka.

24 Mtima wace ulimba ngati mwala, Inde ulimba ngati mwala wa mphero,

25 Ikanyamuka, amphamvu acita mantha; Cifukwa ca kuopsedwa azimidwa nzeru.

26 Munthu akaiyamba ndi lupanga, ligoma; Ngakhale nthungo, kapena mubvi, kapena mkondo.

27 Citsulo iciyesa phesi, Ndi mkuwa ngati mtengo woola.

28 Mubvi suithawitsa, Miyala ya pacoponyera iisandutsa ciputu,

29 Zibonga ziyesedwa ciputu, Iseka kuthikuza kwace kwa nthungo,

30 Kumimba kwace ikunga mapale akuthwa, Itasalala kuthope ngati copunthira.

31 Icititsa nthubwinthubwi pozama ngati nkhali, Isanduliza nyanja ikunge mafuta.

32 Icititsa mifunde yonyezimira pambuyo pace; Munthu akadati pozama pali ndi imvi.

33 Pa dziko lapansi palibe cina colingana nayo, Colengedwa copanda mantha.

34 Ipenya ciri conse codzikuza, Ndiyo mfumu ya zodzitama zonse.

42

1 Pamenepo Yobu anayankha Mulungu, nati,

2 Ndidziwa kuti mukhoza kucita zonse, Ndi kuti palibe coletsa colingirira canu ciri conse,

3 Ndani uyu abisa uphungu wosadziwa kanthu? Cifukwa cace ndinafotokozera zimene sindinazizindikira, Zondidabwiza, zosazidziwa ine,

4 Tamveranitu, ndidzanena ine, Ndidzakufunsani, mundidziwitse.

5 Kumva ndidamva mbiri yanu, Koma tsopano ndikupenyani maso;

6 Cifukwa cace ndekha ndidzinyansa, ndi kulapa M'pfumbi ndi mapulusa.

7 Kunali tsono atanena Yehova mau awa kwa Yobu, Yehova anati kwa Elifazi wa ku Temani, Mkwiyo wanga wakuyakira iwe ndi mabwenzi ako awiri, pakuti simunandinenera coyenera monga ananena mtumiki wanga Yobu.

8 Ndipo tsono, mudzitengere ng'ombe zisanu ndi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri, mumuke kwa mtumiki wanga Yobu, mudzifukizire nokha nsembe yopsereza; ndi mtumiki wanga Yobu adzapempherera inu, pakuti ndidzambvomereza iyeyu, kuti ndisacite nanu monga mwa kupusa kwanu; popeza simunandinenera coyenera monga ananena mtumiki Yobu.

9 Namuka Elifazi wa ku Temani, ndi Bilidadi Msuki, ndi Zofara wa ku Naama, nacita monga Yehova adawauza; ndipo Yehova anabvomereza Yobu.

10 Ndipo Yehova anacotsa ukapolo wa Yobu, pamene anapempherera mabwenzi ace; Yehova nacurukitsa zace zonse za Yobu mpaka kuziwirikiza.

11 Pamenepo anamdzera abale ace onse, ndi alongo ace onse, ndi onse odziwana naye kale, nadya naye mkate m'nyumba yace, nampukusira mitu, namtonthoza pa zoipa zonse Yehova anamfikitsirazi; nampatsanso yense ndarama ndi mphete yagolidi.

12 Ndipo Yehova anadalitsa citsiriziro ca Yobu koposa ciyambi cace, ndipo anali nazo nkhosa zikwi khumi ndi zinai, ndi ngamila zikwi zisanu ndi cimodzi, ndi ng'ombe zamagoli cikwi cimodzi, ndi aburu akazi cikwi cimodzi.

13 Anali naonso ana amuna asanu ndi awiri ndi ana akazi atatu.

14 Ndipo anamucha dzina la woyamba Yemima, ndi dzina la waciwiri Keziya, ndi dzina la wacitatu Kerenihapuki.

15 Ndipo m'dziko monse simunapezeka akazi okongola ngati ana akazi a Yobu, nawapatsa colowa atate wao pamodzi ndi alongo ao.

16 Ndipo zitatha izi, Yobu anakhala ndi moyo zaka zana limodzi mphambu makumi anai, naona ana ace ndi zidzukulu zace mibadwo inai.

17 Namwalira Yobu, wokalamba ndi wa masiku ocuruka.