1 MAU a Yehova amene anadza kwa Mika wa ku Morese masiku a Yotamu, Ahazi, ndi Hezekiya, amene adaona za Samariya ndi Yerusalemu.
2 Imvani, mitundu ya anthu, inu nonse; tamvera, dziko lapansi, ndi zonse ziri m'mwemo; ndipo Ambuye Yehova akhale mboni yakutsutsa inu, Ambuye m'Kacisi wace wopatulika.
3 Pakuti, taonani, Yehova alikuturuka m'malo mwace, nadzatsika, nadzaponda pa misanje ya dziko lapansi.
4 Ndi mapiri adzasungunuka pansi pa Iye, ndi zigwa zidzang'ambika, ngati sera pamoto, ngati madzi otsanulidwa potsetseremba.
5 Cicitika ici conse cifukwa ca kulakwa kwa Yakobo, ndi macimo a nyumba ya Israyeli. Kulakwa kwa Yakobo nkotani? Si ndiko Samariya? ndi misanje ya Yuda ndi iti? si ndiyo Yerusalemu?
6 Cifukwa cace ndidzaika Samariya ngati mulu wa miyala ya m'munda, ngati zooka m'munda wamphesa; ndipo ndidzataya miyala yace m'cigwa, ndi kufukula maziko ace.
7 Ndi mafano ace osema onse adzaphwanyika, ndi mphotho zace zonse zidzatenthedwa ndi moto, ndi mafano ace onse ndidzawapasula; pakuti anazisonkhanitsa pa mphotho ya mkazi waciwerewere, ndipo zidzabwerera ku mphotho ya mkazi waciwerewere.
8 Cifukwa ca ici ndidzacita maliro, ndi kucema, ndidzayenda wolandidwa ndi wamarisece; ndidzalira ngati mimbulu, ndi kubuma ngati nthiwatiwa.
9 Pakuti mabala ace ndi osapola; pakuti afikira ku Yuda; afikira ku cipata ca anthu anga, ku Yerusalemu.
10 Musacifotokoza m'Gati, musalira misozi konse; m'nyumba ya Afira ndinagubuduka m'pfumbi.
11 Pitiratu, wokhala m'Safiri iwe, wamarisece ndi wamanyazi; wokhala m'Zanana sanaturuka; maliro a Betezeli adzakulandani pokhala pace.
12 Pakuti wokhala m'Maroti alindira cokoma, popeza coipa catsika kwa Yehova kumka ku cipata ca Yerusalemu.
13 Manga gareta ku kavalo waliwiro, wokhala m'Lakisi iwe, woyamba kucimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni ndi iye; pakuti zolakwa za Israyeli zinapezedwa mwa iwe.
14 Cifukwa cace pereka mphatso zolawirana kwa Moreseti Gati; nyumba za Akizibi zidzakhala cinthu cabodza kwa mafumu a Israyeli.
15 Ndidzakutengeranso wokhala m'Maresa iwe, iye amene adzakulandira ukhale colowa cace; ulemerero wa Israyeli udzafikira ku Adulamu.
16 Udziyeseze wadazi, udzimete wekha cifukwa ca ana ako okondwera nao; kuza dazi lako ngati la muimba; pakuti anakucokera, nalowa ndende.
1 Tsoka iwo akulingirira cinyengo, ndi kukonza coipa pakama pao! kutaca m'mawa acicita, popeza cikhozeka m'manja mwao.
2 Ndipo akhumbira minda, nailanda; ngakhale nyumba, nazicotsa; asautsa mwamuna ndi nyumba yace, inde munthu ndi colowa cace.
3 Cifukwa cace atero Yehova, Taonani, ndilingirira coipa pa banja ili, cimene simudzacotsako makosi anu, kapena kuyenda modzikuza inu; Pakuti nyengo iyi ndi yoipa.
4 Tsiku ilo adzanena fanizo lakunena inu, nadzalira maliro olemerera, ndi kuti, Tapasuka konse; iye asintha gawo la anthu anga; ha! andicotsera ili! agawira opikisana minda yathu.
5 Cifukwa cace udzasowa woponya cingwe camaere m'msonkhano wa Yehova.
6 Musamanenera, amanenera ati. Sadzanenera kwa awa; matonzo sadzacoka.
7 Kodi adzati, Nyumba ya Yakobo iwe, Mzimu wa Yehova waperewera kodi? izi ndi nchito zace kodi? Mau anga samcitira zokoma kodi, iye amene ayenda coongoka?
8 Koma ngakhale dzulo anthu anga anauka ngati mdani; mukwatula copfunda ku maraya a iwo opitirira mosatekeseka, ngati anthu osafuna nkhondo.
9 Muwataya akazi a anthu anga kunja kwa nyumba zao zokondweretsa; mucotsa ulemerero wanga kwa ana ao kosatha.
10 Nyamukani, cokani, pakuti popumula panu si pano ai; cifukwa ca udio Wakuononga ndi cionongeko cacikuru.
11 Munthu akayenda ndi mtima wacinyengo ndi kunama, ndi kuti, Ndidzanenera kwa iwe za vinyo ndi cakumwa cakuledzeretsa; iye ndiye mneneri wa anthu ace.
12 Ndidzakumemezani ndithu, Yakobo, inu nonse; ndidzasonkhanitsa ndithu otsala a Israyeli; ndidzawaika pamodzi ngati nkhosa za ku Boma; ngati zoweta pakati pa busa pao adzacita phokoso cifukwa ca kucuruka anthu.
13 Wotyola wakwera pamaso pao; iwo anatyola, napita kucipata, naturuka pomwepo; ndi mfumu yao yapita pamaso pao, ndipo Yehova awatsogolera.
1 Ndipo ndinati, Imvanitu, inu akuru a Yakobo, ndi oweruza a nyumba ya Israyeli; simuyenera kodi kudziwa ciweruzo?
2 inu amene mudana naco cokoma ndi kukondana naco coipa; inu akumyula khungu lao pathupi pao, ndi mnofu wao pa mafupa ao;
3 inu amene mukudyanso mnofu wa anthu anga; ndi kusenda khungu lao ndi kutyola mafupa ao; inde awaduladula ngati nyama yoti aphike, ndi ngati nyama ya mumphika.
4 Pamenepo adzapfuulira kwa Yehova, koma sadzawayankha; inde, adzawabisira nkhope yace nthawi yomweyo, monga momwe anaipsa macitidwe ao.
5 Atero Yehova za aneneriakulakwitsa anthu anga; akuluma ndi mano ao, ndi kupfuula, Mtendere; ndipo, ali yense wosapereka m'kamwa mwao, amkonzera nkhondo;
6 cifukwa cace kudzakhala ngati usiku kwa inu, wopanda masomphenya; ndipo kudzadera inu, wopanda kulosa; ndi dzuwa lidzalowera aneneri, ndi usana udzawadera bii.
7 Ndipo alauli adzacita manyazi, ndi olosa adzathedwa nzeru; ndipo onsewo adzasunama; pakuti kuyankha kwa Mulungu kulibe.
8 Koma ine ndidzala nayo mphamvu mwa Mzimu ya Yehova, ndi ciweruzo, ndi camuna, kufotokozera Yakobo kulakwa kwace, ndi kwa Israyeli cimo lace.
9 Tamvanitu ici, akuru a nyumba ya Yakobo inu, ndi oweruza a nyumba ya Israyeli inu, akuipidwa naco ciweruzo, ndi kupotoza zoongoka zonse.
10 Amanga Ziyoni ndi mwazi, ndi Yerusalemu ndi cisalungamo.
11 Akuru ace aweruza cifukwa ca mphotho, ndi ansembe ace aphunzitsa cifukwa ca malipo, ndi aneneri ace alosa cifukwa ca ndarama; koma atsamira pa Yehova, nati, Kodi Yehova sali pakati pa ife? palibe coipa codzatigwera.
12 Momwemo Ziyoni adzalimidwa ngati: munda cifukwa ca inu, ndi m'Yerusalemu mudzasanduka miunda, ndi phiri la nyumba ngati misanje ya m'nkhalango.
1 Koma kudzacitika masiku otsiriza, kuti phiri la nyumba ya Yehova lidzakhazikika pamwamba pa mapiri, nilidzakuzika pamwamba pa zitunda; ndi mitundu ya anthu idzayendako.
2 Ndipo amitundu ambiri adzamuka, nadzati, Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova, ndi ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo; kuti Iye atiphunzitse njira zace, ndipo tidzayenda m'mabande ace; pakuti ku Ziyoni kudzaturuka cilamulo, ndi ku Yerusalemu mau a Yehova.
3 Ndipo Iye adzaweruza mwa mitundu yambiri ya anthu, nadzadzudzula amitundu amphamvu ali kutali; ndipo iwo adzasula malupanga ao akhale makasu, ndi mikondo yao ikhale mazenga, mtundu wa anthu sudzasamulira mtundu unzace lupanga, kapena kuphunziranso nkhondo.
4 Koma adzakhala munthu yense patsinde pa mpesa wace, ndi patsinde pa mkuyu wace; ndipo sipadzakhala wakuwaopsa; pakuti pakamwa pa Yehova wa makamu padanena.
5 Pakuti mitundu yonse ya anthu idzayenda, wonse m'dzina la mlungu wace, ndipo ife tidzayenda m'dzina la Yehova Mulungu wathu ku nthawi yomka muyaya.
6 Tsiku ilo, ati Yehova, ndidzamemeza wakutsimphinayo, ndi kusonkhanitsa wopitikitsidwayo, ndi iye amene ndinamsautsa;
7 ndipo wotsimphinayo ndidzamuyesa wotsala, ndi iye wotayidwa kutali mtundu wamphamvu; ndipo Yehova adzakhala mfumu yao m'phiri la Ziyoni kuyambira pamenepo kufikira kosatha.
8 Ndipo iwe, nsanja ya nkhosa, citunda ca mwana wamkazi wa Ziyoni, udzafikira iwe, inde udzafika ulamuliro wakale, ufumu wa mwana wamkazi wa Yerusalemu.
9 Tsono upfuulitsa cifukwa ninji? palibe mfumu mwa iwe kodi? watayika kodi mu uphungu wako, kuti zowawa zakugwira ngati mkazi wobala?
10 Imva zowawa, nuyesetse kubala, mwana wamkazi wa Ziyoni, ngati mkazi wakubala; pakuti udzaturuka m'mudzi tsopano, nudzakhala kuthengo, nudzafika ku Babulo; komweko udzapulumutsidwa; komweko Yehova adzakuombola m'manja a adani ako.
11 Ndipo tsopano amitundu ambiri asonkhana kuyambana nawe, akuti, Aipsidwe, diso lathu lipenye ku Ziyoni.
12 Koma sadziwa zolingirira za Yehova, kapena kuzindikira uphungu wace; pakuti anawasonkhanitsa ngati mitolo kudwale.
13 Nyamuka nupunthe, mwana wamkazi wa Ziyoni; pakuti ndidzasanduliza nyanga yako ikhale yacitsulo, ndi ziboda zako zikhale zamkuwa; ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu; ndipo uzipereka ciperekere phindu lao kwa Yehova, ndi cuma cao kwa Ambuye wa dziko lonse lapansi.
1 Uzisonkhana tsopano magulu magulu, mwana wamkazi wa magulu iwe; watimangira misasa, adzapanda woweruza wa Israyeli ndi ndodo patsaya.
2 Koma iwe, Betelehemu Efrata, ndiwe wamng'ono kuti ukhale mwa zikwi za Yuda, mwa iwe mudzanditurukira wina wakudzakhala woweruza m'Israyeli; maturukiro ace ndiwo a kale lomwe, kuyambira nthawi yosayamba.
3 Cifukwa cace Iye adzawapereka kufikira nthawi yoti wobalayo wabala; pamenepo otsala a abale ace adzabwera pamodzi ndi ana a Israyeli,
4 Ndipo adzaimirira, nadzadyetsa nkhosa zace mu mphamvu ya Yehova, m'ukulu wa dzina la Yehova Mulungu wace; ndipo iwo adzakhalabe; pakuti pamenepo Iye adzakhala wamkuru kufikira malekezero a dziko lapansi.
5 Ndipo ameneyo adzakhala Mtendere; pamene a ku Asuri adzalowa m'dziko lathu, ndi pamene adzaponda m'zinyumba zathu, tidzawaukitsira abusa asanu ndi awiri, ndi akalonga asanu ndi atatu.
6 Ndipo iwo adzatha dziko la Asuri ndi lupanga, ndi dziko la Nimrodi, ndilo polowera pace; ndipo adzatilanditsa kwa a ku Asuri pamene alowa m'dziko lathu, pamene aponda m'kati mwa malire athu.
7 Ndipo otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu, ngati mame ocokera kwa Yehova, ngati mvula paudzu, yosacedwera munthu, yosalindira ana a anthu.
8 Ndipo, otsala a Yakobo adzakhala mwa amitundu, pakati pa mitundu yambiri ya anthu, ngati mkango mwa nyama za kuthengo, ngati msona wa mkango mwa magulu a nkhosa; umenewo ukapitako, upondereza, numwetula, ndipo palibe wakupulumutsa.
9 Dzanja lako likwezeke pamwamba pa iwo akuyambana nawe, ndi adani ako onse aonongeke.
10 Ndipo kudzacitika tsiku ilo, ati Yehova, ndidzaononga akavalo ako m'kati mwako, ndi kutha magareta ako;
11 ndipo ndidzaononga midzi ya m'dziko lako, ndi kupasula malinga ako onse;
12 ndipo ndidzaononga zanyanga za m'dzanja lako; ndipo sudzakhalanso nao alosi;
13 ndidzaononganso mafano ako osema, ndi zoimiritsa zako pakati pako; ndipo sudzalambiranso nchito za manja ako.
14 Ndipo ndidzazula zifanizo zako m'kati mwako, ndi kutha midzi yako.
15 Ndipo ndidzabwezera amitundu osamvera cilango mu mkwiyo waukali.
1 Tamverani tsono conena Yehova: Nyamuka, tsutsana nao mapiri, ndi zitunda zimve mau ako.
2 Tamvani, mapiri inu, citsutsano ca Yehova, ndi inu maziko olimba a dziko lapansi; pakuti Yehova ali naco citsutsano ndi anthu ace, ndipo adzatsutsana ndi Israyeli.
3 Anthu anga inu, ndakucitirani ciani? ndakulemetsani ndi ciani? citani umboni wonditsutsa.
4 Pakuti ndinakukwezani kukuturutsani m'dziko la Aigupto, ndi kuombola inu m'nyumba ya ukapolo; ndipo ndinatuma akutsogolereni Mose, Aroni, ndi Miriamu.
5 Anthu anga, kumbukilanitu cofunsira Balaki mfumu ya Moabu, ndi comuyankha Balamu mwana wa Beori, kuyambira ku Sitimu kufikira ku Giligala; kuti mudziwe zolungama za Yehova.
6 Ndidzafika kwa Yehova ndi ciani, ndi kuwerama kwa Mulungu Wam'mwamba? Kodi ndifike kwa Iye ndi nsembe zopsereza, ndi ana a ng'ombe a caka cimodzi?
7 Kodi Yehova adzakondwera nazo nkhosa zamphongo zikwi, kapena ndi mitsinje ya mafuta zikwi khumi? Kodi ndipereke mwana wanga woyamba cifukwa ca kulakwa kwanga, cipatso ca thupi langa cifukwa ca kucimwa kwa moyo wanga?
8 Iye anakuuza, munthuwe, comwe ciri cokoma; ndipo Yehova afunanji nawe koma kuti ucite colungama, ndi kukonda cifundo ndi kuyenda modzicepetsa ndi Mulungu wako?
9 Mau a Yehova aitana mudzi, ndi wanzeru aopa dzina lanu; tamverani ndodo, ndi Iye amene anaiika.
10 Kodi m'nyumba ya woipa mukali cuma cosalungama, ndi muyeso wocepa umene ayenera kuipidwa nao?
11 Kodi ndikhoza kuyera ndi miyeso yoipa, ndi thumba la miyala yonyenga?
12 Pakuti anthu ace olemera adzala ndi ciwawa, ndi okhalamo amanena bodza, ndi lilime lao limacita monyenga m'kamwa mwao.
13 Cifukwa cace Inenso ndakukantha ndi kukupweteketsa; ndakupulula cifukwa ca zocimwa zako.
14 Udzadya koma osakhuta; ndi njala yako idzakhala pakati pako; ndipo udzacotsa koma osalanditsa; ndi ici wacilanditsa ndidzacipereka kulupanga.
15 Udzafesa koma osaceka; udzaponda azitona koma osadzola mafuta; udzaponda mphesa koma osamwa vinyo.
16 Pakuti asunga malemba a Omri, ndi nchito za nyumba ya Ahabu, ndipo mumayenda m'uphungu wao; kuti ndikusandulize bwinja, ndi okhalamo cotsonya; ndipo mudzasenza citonzo ca anthu anga.
1 Kalanga ine! pakuti ndikunga atapulula zipatso za m'mwamvu, atakunkha m'munda wamphesa; palibe mphesa zakudya; moyo wanga ukhumba nkhuyu yoyamba kupsa.
2 Watha wacifundo m'dziko, palibe woongoka mwa anthu; onsewo alalira mwazi; yense asaka mbale wace ndi ukonde.
3 Manja ao onse awiri agwira coipa kucicita ndi cangu; kalonga apempha, ndi woweruza aweruza cifukwa ca mphotho; ndi wamkuruyo angonena cosakaza moyo wace; ndipo aciluka pamodzi.
4 Wokoma wa iwo akunga mitungwi; woongoka wao aipa koposa mpanda waminga; tsiku la alonda ako la kulangidwa kwako lafika, tsopano kwafika kuthedwa nzeru kwao.
5 Musakhulupirira bwenzi, musatama bwenzi loyanja; usamtsegulire pakhomo pakamwa pako, ngakhale kwa iye wogona m'fukato mwako.
6 Pakuti mwana wamwamuna apeputsa atate, mwana wamkazi aukira amace, mpongozi aukira mpongozi wace; adani ace a munthu ndiwo a m'nyumba yace.
7 Koma ine, ndidzadikira Yehova; ndidzalindirira Mulungu wa cipulumutso canga; Mulungu wanga adzandimvera.
8 Usandiseka, mdani wangawe; pakugwa ine ndidzaukanso; pokhala ine mumdima Yehova adzakhala kuunika kwanga.
9 Ndidzasenza mkwiyo wa Yehova, cifukwa ndamcimwira, mpaka andinenera mlandu wanga, ndi kundiweruzira mlandu wanga; adzanditurutsira kwa kuunika, ndipo ndidzapenya cilungamo cace.
10 Pamenepo mdani wanga adzaciona, ndi manyazi adzamkuta iye amene adati kwa ine, Ali kuti Yehova Mulungu wako? Maso anga adzamuona; tsopano adzampondereza ngati thope la m'miseu.
11 Tsiku lakumanga malinga ako, tsiku lomwelo lembalo lidzacotsedwa kunka kutali.
12 Tsiku lomwelo adzadza kwa iwe, kucokera ku Asuri ndi midzi ya ku Aigupto, kuyambira ku Aigupto kufikira ku Mtsinje, ndi kuyambira kunyanja kufikira kunyanja, ndi kuyambira kuphiri kufikira kuphiri.
13 Koma dziko lidzakhala labwinja cifukwa ca iwo okhalamo, mwa zipatso za macitidwe ao.
14 Mudyetse anthu anu ndi ndodo yanu, nkhosa za colowa canu zokhala pa zokha m'nkhalango pakati pa Karimeli, zidye m'Basana ndi m'Gileadi masiku a kale lomwe.
15 Monga masiku a kuturuka kwako m'dziko la Aigupto ndidzamuonetsa zodabwitsa.
16 Amitundu adzaona nadzacita manyazi ndi mphamvu yao yonse; adzagwira pakamwa, m'makutu mwao mudzagontha.
17 Adzanyambita pfumbi ngati njoka; ngati zokwawa za padziko, adzanjenjemera poturuka m'ngaka mwao; adzafika kwa Yehova Mulungu wao ndi mantha, nadzaopa cifukwa ca iwe.
18 Ndani Mulungu wofanana ndi Inu, wakukhululukira mphulupulu, wakupitirira zolakwa za otsala a colowa cace? sasunga mkwiyo wace ku nthawi yonse popeza akondwera naco cifundo.
19 Adzabwera, nadzaticitira nsoni; adzagonjetsa mphulupulu zathu; ndipo mudzataya zocimwa zao zonse m'nyanja yakuya,
20 Mudzapatsa kwa Yakobo coonadi, ndi kwa Abrahamu cifundo cimene munalumbirira makolo athu kuyambira masiku a kale lomwe.