1

1 PAULO, woitanidwa akhale mtumwi wa Yesu Kristu mwa cifuniro ca Mulungu, ndi Sositene mbaleyo,

2 kwa Mpingo wa Mulungu wakukhala m'Korinto, ndiwo oyeretsedwa mwa Kristu Yesu, oitanidwa akhale oyera mtima, pamodzi ndi onse akuitana pa dzina la Ambuye wathu Yesu Kristu, m'malo monse, ndiye wao, ndi wathu:

3 Cisomo kwa inu ndi mtendere zocokera kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Kristu.

4 Ndiyamika Mulungu wanga nthawi yonse kaamba ka inu, cifukwa ca cisomo ca Mulungu cinapatsidwa kwa inu mwa Kristu Yesu;

5 kuti m'zonse muoalemezedwa mwa iye, m'mau onse, ndi cidziwitso conse;

6 mongaumboni wa Kristu unakhazikika mwa inu;

7 kotero kuti sicikusowani inu caufuru ciri conse; pakulindira inu bvumbulutso la Ambuye wathu Yesu Kristu;

8 amenenso adzakukhazikitsani inu kufikira cimariziro, kuti mukhale opanda cifukwa m'tsiku la Ambuye: wathu Yesu Kristu.

9 Mulungu ali, wokhulupirika amene munaitanidwa mwa iye, ku ciyanjano ca Mwana wace Yesu Kristu, Ambuye wathu.

10 Koma ndikudandaulirani inu, abale, mwa dzina la Ambuye wathu Yesu Kristu, kuti munene cimodzimodzi inu nonse, ndi kuti pasakhale malekano pakati pa inu; koma mumangike mu mtima womwewo ndi m'ciweruziro comweco.

11 Pakuti zinamveka kwa ine za inu, abale anga, ndi iwo a kwa Kloe, kuti pali makani pakati pa inu.

12 Koma ici ndinena, kuti yense wa inu anena, Ine ndine wa Paulo; koma ine wa Apolo; koma ine wa Kefa; koma ine wa Kristu.

13 Kodi Kristu wagawika? Kodi Paulo anapacikidwa cifukwa ca inu? Kapena kodi munabatizidwa m'dzina la Paulo?

14 Ndiyamika Mulungu kuti sindinabatiza mmodzi yense wa inu, koma Krisipo ndi Gayo;

15 kuti anganene mmodzi kuti mwabatizidwa m'dzina langa.

16 Koma ndinabatizanso a pa banja la Stefana; za ena, sindidziwa ngati ndinabatiza wina yense.

17 Pakuti Kristu sanandituma ine kubatiza, koma kulalikira Uthenga Wabwino, si mu nzeru ya mau, kuti mtanda wa Kristu ungayesedwe wopanda pace.

18 Pakuti mau a mtanda ali ndithu cinthu copusa kwa iwo akutayika, koma kwa ife amene tirikupulumutsidwa ali mphamvu ya Mulungu.

19 Pakuti kulembedwa, Ndidzaononga nzeru za anzeru, Ndi kucenjerakwa ocenjera odidzakutha.

20 Ali kuti wanzeru? Mlembi ali kuti? Ali kuti wotsutsana wa nthawi ya pansi pano? Kodi Mulungu sanaipusitsa nzeru ya dziko lapansi?

21 Pakuti popeza m'nzeru ya Mulungu dziko lapansi, mwa nzeru yace, silinadziwa Mulungu, cidamkonda Mulungu kupulumutsa okhulupirawo mwa copusa ca kulalikira.

22 Ndipo popeza Ayuda afunsa zizindikilo, ndi Ahelene atsata nzeru:

23 koma ife tilalikira Kristu wopacikidwa, kwa Ayudatu cokhumudwitsa, ndi kwa amitundu cinthu copusa;

24 koma kwa iwo oitanidwa, ndiwo Ayuda ndi Ahelene, Kristu 1 mphamvu ya Mulungu, ndi 2 nzeru ya Mulungu.

25 Cifukwa kuti copusa ca Mulungu ciposa anthu ndi nzeru zao; ndipo cofoka ca Mulunguciposa anthu ndi mphamvu yao.

26 Pakuti penyani maitanidwe anu, abale, kuti 3 saitanidwa ambiri anzeru, monga mwa thupi; ambiri amphamvu, mfulu zambiri, iai;

27 koma 4 Mulungu anasankhula zopusa za dziko lapansi, kuti akacititse manyazi anzeru; ndipo zofoka za dziko lapansi Mulungu anazisankhula, kuti akacititse manyazi zamphamvu;

28 ndipo zopanda pace za dziko lapansi, ndi zonyozeka, anazisankhula Mulungu, ndi zinthu zoti kulibe; 5 kuti akathere zinthu zoti ziriko;

29 6 kuti thupi liri lonse lisadzitamande pamaso pa Mulungu.

30 Koma kwa iye muli inu mwa Kristu Yesu, 7 amene anayesedwa kwa ife nzeru ya kwa Mulungu, ndi cilungamo ndi ciyeretso ndi ciombolo;

31 kuti monga mwalembedwa, iye amene adzitamanda, adzitamande mwa Ambuye.

2

1 Ndipo ine, abale, m'mene ndinadza kwa inu, sindinadza ndi kuposa kwa mau, kapena kwa nzeru, polalikira kwa inu cinsinsi ca Mulungu.

2 Pakuti ndinatsimikiza mtima kuti ndisadziwe kanthu mwa inu koma Yesu Kristu, ndi iye wopacikidwa.

3 Ndipo ine ndinakhala nanu mofoka ndi m'mantha, ndi monthunthumira mwambiri.

4 Ndipo mau anga ndi kulalikira kwanga sanakhala ndi mau okopa a nzeru, koma m'cionetso ca Mzimu ndi ca mphamvu;

5 kuti cikhulupiriro canu cisakhale m'nzeru ya anthu, koma mu mphamvu ya Mulungu.

6 Koma tilankhula nzeru mwa angwiro; koma si nzeru ya nthawi yino ya pansi pano, kapena ya akulu a nthawi yino ya pansi pano, amene alinkuthedwa;

7 koma tilankhula nzeru ya Mulungu m'cinsinsi, yobisikayo, imene Mulungu anaikiratu, pasanakhale nyengo za pansi pano, ku ulemerero wathu,

8 imene saidziwa mmodzi wa akulu a nthawi a pansi pano; pakuti akadadziw sakadapaeika Mbuye wa ulemerero

9 koma monga kulembedwa, Zimene diso silinaziona, ndi khutu silinazimva, Nisizinalowa mu mtima wa munthu, Zimene ziri zonse Mulungi anakonzereratu iwo aku mkonda iye.

10 Koma kwa ife Mulungu anati onetsera izi mwa Mzimu; pakuti Mzimu asanthula zonse, zakuya za Mulungu zomwe.

11 Pakuti ndani wa anthu adziwa za munthu, koma mzimu wa munthuyu uli mwa iye? momwemonso za Mulungu palibe wina azidziwa, koma Mzimu wa Mulungu.

12 Koma sitinalandira ife mzimu wa dziko lapansi, koma Mzimu wa kwa Mulungu, kuti tikadziwe zimene zipatsidwa kwa ife ndi Mulungu kwaufulu.

13 Zimenenso tilankhula, si ndi mau ophunzitsidwa ndi nzeru za munthu, koma ophunzitsidwa ndi Mzimu; ndi kulinganiza zamzimu ndi zamzimu.

14 Koma munthu wa cibadwidwe ca umunthu salandira za Mzimu wa Mulungu: pakuti aziyesa zopusa; ndipo sakhoza kuzizindikira, cifukwa ziyesedwa mwauzimu.

15 Koma iye amene ali wauzimu ayesa zonse, koma iye yekha sayesedwa ndi mmodzi yense.

16 Pakuti wadziwa ndani mtima wa Ambuye, kuti akamlangize iye? Koma ife tiri nao mtima wa Kristu.

3

1 Ndipo ine, abale, sindinakhoza kulankhula ndi inu manga ndi auzimu, koma monga athupi, monga makanda mwa Kristu.

2 Ndinaiyetsa inu mkaka, si cakudya colimba ai; pakuti simunaeikhoza; ngakhale tsopano lino simucikhoza; pakuti mulinso athupi;

3 pakuti, pokhala pali nkhwidzi ndi ndeu pakati pa inu simuli athupi kodi, ndi kuyendayenda monga mwa munthu?

4 Pakuti pamene wina anena, ine ndine wa Paulo; koma mnzace, Ndine wa Apolo; simuli anthu kodi?

5 Ndipo Apolo nciani, ndi Paulo nciani? Atumiki amene munakhulupirira mwa iwo, yense monga Ambuye anampatsa.

6 Ndinanka ine, anathirira Apolo; kama Mulungu anakulitsa.

7 Cotero sali kanthu kapena wookayo, kapena wothirirayo; kama Mulungu amene akulitsa.

8 Koma wookayo ndi wothirirayoali amodzi; koma yense adzalandira mphotho yace ya iye yekha, monga mwa kucititsa kwace kwa iye yekha.

9 Pakuti ife ndife anchito anzace a Mulungu; cilimo ca Mulungu, cimango ca Mulungu ndi inu.

10 Monga mwa cisomo ca Mulungu cidapatsidwa kwa ine, ngati mwini mamangidwe waluso, ndinaika maziko, koma wina amangapo. Koma yense ayang'anire umo amangira pamenepo.

11 Pakuti palibe munthu akhoza kuika maziko ena, koma amene aikidwako, ndiwo Yesu Kristu.

12 Koma ngati wina amanga pa mazikowo, golidi, siliva, miyala va mtengo wace, mtengo, maudzu, dziputu,

13 nchito ya yense idzaonetsedwa; pakuti tsikulo lidzaisonyeza, cifukwa kuti yabvumbuluka m'moto; ndipo mota wokha udzayesera nchito ya yense ikhala yotani.

14 Ngati nchito ya munthu ali yense khala imene anaimangako, adzaandira mphotho.

15 Ngati nchito ya wina itenthedwa, zidzaonongeka zace; koma iye yekha adzapulumutsilwa; koma monga momwe mwa noto.

16 Kodi simudziwa kuti muli Kacisi wa Mulungu, ndi kuti Mzimu wa Mulungu agonera mwa inu?

17 Ngati wina aononga kacisi wa Mulungu, ameneyo Mulungu adzamuononga; pakuti kacisi wa Mulungu ali wopatulika, ameneyo ndi inu.

18 Munthu asadzinyenge yekha; igati winaayesa kuti ali wanzeru nwa inu m'nthawi yino ya pansi iano, akhale wopusa, kuti akakhale vanzeru.

19 Pakuti nzeru ya dziko ina lapansi iri yopusa kwa Mulungu, Pakuti, kwalembedwa, iye agwira mzeru m'cenjerero lao;

20 ndiponso Ambuye azindikira zolingirira za mzeru, kuti ziri zopanda pace.

21 Cifukwa cace palibemmodzi adziamande mwa anthu. Pakuti zinthu onse nzanu;

22 ngati Paulo, kapena Apolo, kapena Kefa, kapena dziko apansi, kapena moyo, kapena imfa, capena za makono ano, kapena drinkudza; zonse ndi zanu;

23 kona inu ndinu a Kristu; ndi Kristu ndiye wa Mulungu.

4

1 Cotero munthu atiyese ife, monga atumiki a Kristu, ndi adindo a zinsinsi za Mulungu.

2 Komatu pano pafunika za adindo, kuti munthu akhale wokhulupirika.

3 Koma kwa ine kuli kanthu kakang'ono ndithu, kuti ndiweruzidwe ndi Inu, kapena pa bwalo la munthu; koma sindiweruza ngakhale ndekha.

4 Pakuti sindidziwa kanthu kakundiparamulitsa; koma m'menemo sindiyesedwa wolungama; koma wondiweruza ine ndiye Ambuye.

5 Cifukwa cace musaweruze kanthu isanadze nthawi yace, kufikira akadze Ambuye, amenenso adzaonetsera zobisika za mdima, nadzasonyeza zitsimikizo za mtima; ndipo pamenepo yense adzakhala nao uyamiko wace wa kwa Mulungu.

6 Koma izi, abale, ndadziphiphiritsira ndekha ndi Apolo, cifukwa ca inu, kuti mwa ife mukaphunzire kusapitirira zimene zilembedwa; kuti pasakhale mmodzi wodzitukumulira mnzace ndi kukana wina.

7 Pakuti akusiyanitsa iwe ndani? Ndipo uli naco ciani cosati wacilandira? Koma ngati wacilandira udzitamanda bwanji, monga ngati sunacilandira?

8 M wadzala kale, mwalemerera kale, mwacita ufumu opanda ife; ndipo mwenzi mucitadi ufumu, kuti ifenso tikacite ufumu pamodzi ndi inu.

9 Pakuti ndiyesa, kuti Mulungu anaoneketsa ife atumwi otsiriza, monga titi tife; pakuti takhala ife coonetsedwa ku dziko lapansi, ndi kwa angelo, ndi kwa anthu.

10 Tiri opusa ife cifukwa ca Kristu, koma muli ocenjera inu mwa Kristu; tiri ife ofoka, koma inu amphamvu; inu ndinu olemekezeka, koma ife ndife onyozeka.

11 Kufikira nthawi yomwe yino timva njala, timva ludzu, tid amarisece, tikhomedwa, tiribe pokhazikika;

12 ndipo tigwiritsa nchito, ndi kucita ndi manja athu a ife tokha; polalatidwa tidalitsa; pozunzidwa, tipirira;

13 ponamizidwa, tipempha; takhala monga zonyansa za dziko lapansi, litsiro la zinthu zonse, kufikira tsopano,

14 Sindilembera izi kukucititsani manyazi, koma kucenjeza inu monga ana anga okondedwa.

15 Pakuti mungakhale muli nao aphunzitsi zikwi khumi mwa Kristu, mulibe atate ambiri; pakuti mwa Kristu Yesu ine ndinabala Inu mwa Uthenga Wabwino.

16 Cifukwa cace ndikupemphani, khalani akutsanza ine.

17 Cifukwa ca ici ndatuma kwa inu Timoteo, ndiye mwana wanga wokondedwa ndi wokhulupirika mwa Ambuye, amene adzakumbutsa inu njira zanga za mwa Kristu, monga ndiphunzitsa ponsepom'Mipingo yonse.

18 Koma ena adzitukumula, monga ngati sindinalinkudza kwa inu.

19 Koma ndidzafika kwa inu msanga, akandilola Ambuye; ndipo ndidzazindikira si mau a iwo odzitukumula, koma mphamvuyi.

20 Pakuti ufumu wa Mulungu suli m'mau, koma mumphamvu, Mufuna ciani?

21 Kodi ndifike kwa inu ndi ndodo, kapena mwacikondi, ndi mzimu wakufatsa?

5

1 Kwamveka ndithu kuti kuli cigololo pakati pa inu, ndipo cigololo cotere conga sicimveka mwa amitundu, kuti wina ali naye mkazi wa atate wace.

2 Ndipo mukhala odzitukumula, kosati makamaka mwacita cisoni, kuti acotsedwe pakati pa inu iye amene anacita nchito iyi.

3 Pakuti inedi, thupi langa kulibe, koma mzimu wanga ulipo, ndaweruza kale, monga ngati ndiripo,

4 m'dzina la Ambuye wathu Yesu, posonkhana pamodzi inu ndi mzimu wanga, ndi mphamvu ya Ambuye wathu Yesu,

5 kumpereka iye wocita cotere kwa Satana, kuti lionongeke thupi, kuti mzimu upulumutsidwe m'tsiku la Ambuye Yesu.

6 Kudzitamanda kwanu sikuli bwino. Kodi simudziwa kuti cotupitsa pang'ono citupitsa mtanda wonse?

7 Tsukani cotupitsa cakale, kuti mukakhale mtanda watsopano, monga muli osatupa. Pakutinso Paskha wathu waphedwa, ndiye Kristu;

8 cifukwa cace ticita phwando, si ndi cotupitsa cakale, kapena ndi cotupttsaca dumbo, ndi kuipa mtima, koma ndi mkate wosatupa wa kuona mtima, ndi coonadi.

9 Ndinalembera inu m'kalata uja, kuti musayanjane ndi acigololo;

10 si konse konse ndi acigololo a dziko lino lapansi, kapena ndi osirira, ndi okwatula, kapena ndi opembedza mafano; pakuti nkutero mukaturuke m'dziko lapansi;

11 koma tsopano ndalembera inu kuti musayanjane naye, ngati wina wochedwa mbale ali wacigololo, kapena wosirira, kapena wopembedza mafano, kapena wolalatira, kapena woledzera, kapena wolanda, kungakhale kukadya naye wotere, iai.

12 Pakuti nditani nao akunja kukaweruza iwo? Kodi amene ali m'katimosimuwaweruza ndi inu,

13 komaakunia awaweruza Mulungu? Cotsani woipayo pakati pa inu nokha.

6

1 Kodiakhoza winawa inu, pamene ali nao mlandu pa mnzace, kupita kukaweruzidwa kwa osalungama, osati kwa oyera mtima?

2 Kapena kodi simudziwa kuti oyera mtima adzaweruza dziko lapansi? Ndipo ngati dziko lapansi liweruzidwa ndi inu, muli osayenera kodi kuweruza timilandu tocepacepa?

3 Kodi simudziwa kuti tidzaweruza angelo? koposa kotani nanga zinthu za moyo uno?

4 Cifukwa cace, ngati muli nayo mirandu ya zinthu za moyo uno, kodi muweruzitsa iwo amene ayesedwa acabe mu Mpingo?

5 Ndinena ici kukucititsani inu manyazi. Kodi nkutero kuti mwa inu palibe mmodzi wanzeru, amene adzakhoza kuweruza pa abale,

6 koma mbale anena mlandu ndi mbale, ndikotu kwa osakhulupira?

7 Koma pamenepo pali cosowa konse konse mwa inu, kuti muli nayo mirandu wina ndi mnzace. Cifukwa ninji simusankhula kulola kuipsidwa? simusankhula cifukwa ninji kulolakunyengedwa?

8 Koma muipsa, nimunyenga, ndipo mutero nao abale anu.

9 Kapenasimudziwa kuti osalungama sadzalandira ufumu wa Mulungu? Musasoceretsedwe; adama, kapena opembedza mafano, kapena acigololo, kapena olobodoka ndi zoipa, kapena akudziipsa ndi amuna,

10 kapena ambala, kapena osirira, kapena oledzera, kapena olalatira, kapena olanda, sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

11 Ndipo ena ainu munali otere; koma munasambitsidwa, koma munayeretsedwa, koma munayesedwa olungama, m'dzina la Ambuye Yesu Kristu, ndi mwa Mzimu wa Mulungu wathu.

12 Zinthu zonse ziloledwa kwa ine; koma si zonse zipindula, Zinthu zonse ziloledwa kwa ine, koma sindidzalamulidwa naco cimodzi.

13 Zakudya ndizo za mimba, ndi mimba ndiyo ya zakudya; koma Mulungu adzathera iyi ndi izi. Koma thupi siliri la cigololo, koma la Ambuye, ndi Ambuye wa thupi;

14 koma Mulungu anaukitsa Ambuye, ndiponso adzaukitsa ife mwa mphamvu yace.

15 Kodi simudziwa kuti matupi anu ali ziwalo za Kristu? cifukwa cace ndidzatenga ziwalo za Kristu kodi, ndi kuziyesa ziwalo za mkazi waciwerewere? Msatero iai.

16 Kapena simudziwa kuti iye wophatikidwa ndi mkazi waciwerewere ali thupi limodzi? Pakuti, awiriwo, ati, adzakhala thupi limodzi.

17 Koma iye wophatikidwa ndi Ambuye ali mzimu umodzi.

18 Thawani dama. Cimo liri lonse munthu akalicita liri kunja kwa thupi; koma waciwerewere acimwira thupi lace la iye yekha.

19 Kapena simudziwa kuti thupi lanu liri kacisi wa Mzimu Woyera, amene ali mwa inu, amene muli naye kwa Mulungu? Ndipo simukhala a inu nokha.

20 Pakuti munagulidwa ndi mtengo wace wapatali; cifukwa cace lemekezani Mulungu m'thupi lanu.

7

1 Koma za izi munalembazi; kuli bwino kwa munthu kusakhudza mkazi.

2 Koma cifukwa ca madama munthu yense akhale naye mkazi wa iye yekha, ndi mkazi yense akhale naye mwamuna wa iye yekha.

3 Mwamunayo apereke kwa mkazi mangawa ace; koma modzimodzinso mkazi kwa mwamuna.

4 Mkazi alibe ulamuliro wa pa thupi lace la iye yekha, koma mwamuna ndiye; koma momwemonso mwamuna alibe ulamuliro wa pa thupi laiye yekha, koma mkazi ndiye.

5 Musakanizana, koma ndi kubvomerezana kwanu ndiko, kwa nthawi, kuti mukadzipereke kwa kupemphera, nimukakhalenso pamodzi, kuti Satana angakuyeseni, cifukwa ca kusadziletsa kwanu.

6 Koma ici ndinena monga mwa kulola, si monga mwa kulamulira.

7 Koma mwenzi anthu onse akadakhala monga momwe ndiri ine ndekha. Koma munthu yense ali nayo mphatso yace ya iye yekha kwa Mulungu, wina cakuti, wina cakuti.

8 Koma ndinena kwa osakwatira, ndi kwa akazi amasiye, kuti kuli bwino kwa iwo ngati akhala monganso ine.

9 Koma ngati sadziwa kudziletsa, akwatitsidwe; pakuti nkwabwino kukwatira koposa kutentha mtima.

10 Koma okwatitsidwawo ndiwalamulira, si ine ai, koma Ambuye, kuti mkazi asasiye mwamuna,

11 komanso ngati amsiya akhale osakwatiwa, kapena ayanjanitsidwenso ndi mwamunayo, ndipo mwamuna asalekane naye mkazi.

12 Koma kwa otsalawo ndinena ine, si Ambuye, Ngati mbale wina ali naye mkaziwosakhulupira, ndipo iye abvomera mtima kukhala naye pamodzi, asalekane naye.

13 Ndipo mkazi amene ali naye mwamuna wosakhulupira, nabvomera mtima iye kukhala naye pamodzi, asalekane naye mwamunayo.

14 Pakuti mwamuna wosakhulupirayo ayeretsedwa mwa mkaziyo, ndi mkazi wosakhulupira ayeretsedwa mwa mbaleyo; ngati sikukadatero, ana anu akadakhala osakonzeka, koma tsopano akhala oyera.

15 Koma ngati wosakhulupirayo acoka, acoke. M'mirandu yotere samangidwa ukapolo mbaleyo, kapena mlongoyo, Koma Mulungu watiitana ife mumtendere.

16 Pakuti udziwa bwanji mkazi iwe, ngati udzapulumutsa mwamunayo? kapena udziwa bwanji, mwamuna iwe, ngati udzapulumutsa mkazi?

17 Koma, monga Ambuye wagawira kwa yense, monga Mulungu waitana yense, momwemo ayende. Ndipo kotero ndiika m'Mipingo yonse.

18 Kodi waitanidwa wina wodulidwa? Asakhale wosadulidwa. Kodi waitanidwa wina wosadulidwa? Asadulidwe.

19 Mdulidwe ulibe kanthu, ndi kusadulidwa kulibe kanthu, koma kusunga kwa malamulo a Mulungu.

20 Yense akhale m'maitanidwe m'mene anaitanidwamo.

21 Kodi unaitanidwa uli kapolo? Usasamalako; koma ngati ukhozanso kukhala mfulu, cita nako ndiko.

22 Pakuti iye amene anaitanidwa mwa Ambuye, pokhala ali kapolo, ali mfulu ya Ambuye: momwemonso woitanidwayo, pokhala ali mfulu, ali kapolo wa Kristu.

23 Munagulidwa ndi mtengo wace; musakhale akapolo a anthu.

24 Yense, m'mene anaitanidwamo, abate, akhale momwemo ndi Mulungu.

25 Koma kunena za anamwali, ndiribe lamulo la Ambuye; koma ndikuuzani coyesa ine, monga wolandira cifundo kwa Ambuye kukhala wokhulupirika.

26 Cifukwa cace ndiyesa kuti ici ndi cokoma cifukwa ca cibvuto ca nyengo yino, kuti nkwabwino kwa munthu kukhala monga ali.

27 Kodi wamangika kwa mkazi? Usafune kumasuka. Kodi wamasuka kwa mkazi? Usafune mkazi.

28 Koma ungakhale ukwatira, sunacimwa; ndipo ngati namwali akwatiwa, sanacimwa. Koma otere adzakhala naco cisautso m'thupi, ndipo ndikulekani.

29 Koma ici nditi, abale, yafupika nthawi, kuti tsopano iwo akukhala nao akazi akhalebe monga ngati alibe;

30 ndi iwo akulira, monga ngati salira, ndi iwo akukondwera, monga ngati sakondwera; ndi iwo akugula monga ngati alibe kanthu;

31 ndi iwo akucita nalo dziko lapansi, monga ngati osacititsa; pakuti maonekedwe a dziko ili apita.

32 Koma ndifuna kuti mukhale osalabadira iye amene wosakwatira alabadira zinthu za Ambuye, kuti akondweretse Ambuye;

33 koma iye wokwatira alabadira zinthu za dziko lapansi, kuti akondweretse mkazi wace.

34 Ndi mkazi wokwatiwa ndi namwali asiyananso iye wosakwatiwa alabadira za. Ambuye, kuti akhale woyera m'thupi ndi mumzimu; koma wokwatiwayo, alabadira za dziko lapansi, kuti akondweretse mwamunayo.

35 Koma ici ndinena mwa kupindula kwanu kwa inu nokha; sikuti ndikakuchereni msampha, koma kukuthandizani kucita cimene ciyenera, ndi kutsata citsatire Ambuye, opanda coceukitsa.

36 Koma wina akayesa kuti acitira mwana wace wamkazi cosamuyeoera, ngati palikupitirira pa unamwali wace, ndipo kukafunika kutero, acite cimene afuna, sacimwa; akwatitsidwe.

37 Koma iye amene aima wokhazikika mumtima mwace, wopanda cikakamizo, koma ali nao ulamuliro wa pa cifuniro ca iye yekha, natsimikiza ici mumtima mwa iye yekha, kusunga mwana wace wamkazi, adzacita bwino.

38 Cotero iye amene akwatitsa mwana wace wamkazi acita bwino, ndipo iye wosamkwatitsa acita koposa.

39 Mkazi amangika pokhala mwamuna wace ali ndi moyo; koma atamwalira mwamuna ali womasuka, kuti akwatiwe naye amene afuna, koma mwa Ambuye.

40 Koma akhala wokondwera koposa ngati akhala monga momwe ali, monga mwa kuyesa kwanga; ndipo ndiganiza kuti inenso ndiri naye Mzimu wa Mulungu.

8

1 Koma za zoperekedwa nsembe kwa mafano: Tidziwa kuti tid naco cidziwitso tonse. Cidziwitso citukumula, koma cikondicimangirira.

2 Ngati wina ayesa kuti adziwa kanthu sanayambe kudziwa monga ayenera kudziwa.

3 Koma ngati wina akonda Mulungu, yemweyu adziwika ndi iye.

4 Tsono kunena za kudya zoperekedwa nsembe kwa mafano, tidziwa kuti fano siliri kanthu pa dziko lapansi, ndi kuti palibe Mulungu koma mmodzi.

5 Pakuti ngakhalenso iriko yoti yonenedwa milungu, kapena m'mwamba, kapena pa dziko lapansi, monga iriko milungu yambiri, ndi ambuye ambiri;

6 koma kwa ife kuli Mulungu mmodzi, Atate amene zinthu zonse zicokera kwa iye, ndi ire kufikira kwa iye; ndi Ambuye mmodzi Yesu Kristu, amene zinthu zonse ziri mwa iye, ndi ife mwa iye.

7 Komatu cidziwitso siciri mwa onse; koma ena, ozolowera fano kufikira tsopano, adyako monga yoperekedwa nsembe kwa fano; ndipo cikumbu mtima cao, popeza ncofoka, cidetsedwa.

8 Koma cakudya sicitibvomerezetsa kwa Mulungu; kapena ngati sitidya sitisowa; kapena ngati tidya tiribe kupindulako,

9 Koma yang'anirani kuti ulamuliro wanu umene ungakhale cokhumudwitsa ofokawo.

10 Pakuti wina akaona iwe amene uli naco cidziwitso, ulikukhala pacakudya m'kacisi wa fano, kodi cikumbu mtima cace, popeza ali wofoka, sieidzalimbika kudya zoperekedwa nsembe kwa mafano?

11 Pakuti mwa cidziwitso cako wofokayo atayika, ndiye mbale amene Kristu anamfera.

12 Koma pakucimwira abale, ndi kulasa cikumbu mtima cao cofoka, mucimwira kotero Kristu.

13 Cifukwa cace, ngati cakudya cikhumudwitsa mbale wanga, sindidzadya ayama ku nthawi yonse, kuti ndiogakhumudwitse mbale wanga.

9

1 Kodi sindine mfulu? Kodi slndine mtumwi? Kodi sindinaona Yesu Ambuye wathu? Kodi simuli inu nchito yanga mwa Ambuye?

2 Ngati sindiri mtumwi kwa ena, komatu ndiri kwa inu; pakuti cizindikilo ca utumwi wanga ndi inu mwa Ambuye.

3 Codzikanira canga kwa iwoamene andifunsa ine ndi ici:

4 Kodi tiribe ulamuliro wa kudya ndi kumwa?

5 Kodi tiribe ulamuliro wakuyendayenda naye mkazi, ndiye mbale, monganso atumwi ena, ndi abale a Ambuye, ndi Kefa?

6 Kapena kodi ife tokha, Bamaba ndi ine, tiribe ulamuliro wakusagwira nchito?

7 Msilikari ndani acita nkhondo, nthawi iriyonse, nadzifunira zace yekha? Aoka mipesa ndani, osadya cipatso cace? Kapena aweta gulu ndani, osadyamkaka wace wa gululo? Kodi ndilankhula izi monga mwa anthu?

8 Kapena cilamulo sieinenanso zomwezo?

9 Pakuti m'cilamulo ca Mose mwalembedwa, Usapunamitsa ng'ombe pakupuntha iyo dzinthu. Kodi Mulungu asamalira ng'ombe?

10 Kapena acinena ici konse konse cifukwa ca ife? Pakuti, cifukwa ca ife kwalembedwa: popeza wolima ayenera kulima mwa ciyembekezo, ndi wopunthayo acita mwa ciyembekezo ca kugawana nao.

11 Ngati takufeserani inu zauzimu, kodi ncacikuru ngati ife tituta za thupi lanu?

12 Ngati ena ali nao ulamuliro umene pa inu, si ife nanga koposa? Koma sitinacita nao ulamuliro umene; koma timalola zonse, kuti tingacite cocedwetsa kwa Uthenga Wabwino wa Kristu,

13 Kodi simudziwa kuti iwo akutumikira za kacisi amadya za m'Kacisi, ndi iwo akuimirira guwa la nsembe, agawana nalo guwa la nsembe?

14 Comweconso Ambuyeanalamulira kuti iwo amene alalikira Uthenga Wabwino akhale ndi moyo ndi Uthenga Wabwino.

15 Koma ine sindinacita nako kanthu kaizi; ndipo sindilemba izi kuti cikakhale cotero ndi ine; pakuti kundikomera ine kufa, koma wina asayese kwacabe kudzitamanda kwanga.

16 Pakuti ngati ndilalikira Uthenga Wabwino ndiribe kanthu kakudzitamandira; pakuti condikakamiza ndigwidwa naco; pakuti tsoka ine ngati sindilalikira U thenga Wabwino.

17 Pakuti ngati ndicita ici cibvomerere, mphotho ndiri nayo; koma ngati si cibvomerere; anandikhulupirira m'udindo.

18 Mphotho yanga nciani tsono? Kuti pakulalikira Uthenga Wabwino ndiyese Uthenga Wabwino ukhale waulere, kuti ndisaipse ulamuliro wanga wa mu Uthenga Wabwino.

19 Pakuti pokhala ndinali mfulu kwa onse, ndinadzilowetsa ndekha ukapolo kwa onse, kuti ndipindule ocuruka.

20 Ndipo kwa Ayuda ndinakhala monga Myuda, kuti ndipindule Ayuda; kwa iwo omvera lamulo monga womvera lamulo, ngakhale sindinakhala ndekha womvera lamulo, kuti ndipindule iwo omvera malamulo;

21 kwa iwo opanda lamulo monga wopanda lamulo, wosati wakukhala ine wopanda lamulo kwa Mulungu, koma womvera lamulo twa Kristu kuti ndipindule iwo opanda lamulo.

22 Kwa ofoka ndinakhala ngati wofoka, kuti ndipindule ofoka, Ndakhala zonse kwa anthu onse, 1 kuti pali ponse ndikapulumutse ena.

23 Koma ndicita zonse zifukwa ca Uthenga Wabwino, kuti ndikakhale woyanjana nao.

24 Kodi umudztwa kuti iwo akucita makani a Iwiro, athamangadi onse, koma nmodzi alandira mfupo? Motero 2 thamangani, kuti mukalandire.

25 Koma yense wakuyesetsana adzikaniza zonse. Ndipo iwowa atero kuti alandire korona wakubvunda; 3 koma ife wosabvunda.

26 Cifukwa cace ine ndithamanga cotero, si nonga cosinkhasinkha. Ndilimbaaa cotero, si monga ngati kupanda nlengalenga;

27 koma 4 ndipumpuatha thupi langa, ndipo ndiliyesa capolo; kuti, kapena ngakhale rdalalikira kwa ena, 5 ndingakhale votayika ndekha.

10

1 Pakuti sindifuna, kuti mukhale osadziwa, abale, kuti makolo athu onse anali pansi pa mtambo, naoloka nyanja onse;

2 nabatizidwa onse kwa Mose, mumtambo, ndi m'nyanja,

3 nadya onse cakudya cauzimu cimodzimodzi;

4 namwa onse cakumwa cauzimu cimodzimodzi; pakuti anamwa mwa thanthwe lauzimu lakuwatsata; koma thanthwelo ndiye Kristu.

5 Koma ocuruka a iwo Mulungu sanakondwera nao; pakuti anamwazika m'cipululu.

6 Koma zinthu izi zinacitika, zikhale zoticenjeza ife, kuti tisalakalake zoipa ife, monganso iwowo analakalaka.

7 Kapena musakhale opembedza mafano, monga ena a iwo, monga kwalembedwa, Anthu anakhala pansi kudya ndi kumwa, nanyamuka kusewera.

8 Kapena tisacite dama monga ena a iwo anacita dama, nagwa tsiku limodzi zikwi makumi awiri ndi zitatu.

9 Kapena tisayese Ambuye, monga ena a iwo anayesa, naonongeka ndi njoka zija.

10 Kapena musadandaula, monga ena a iwo anadandaula, naonongeka ndi woonongayo.

11 Koma izi zinacitika kwa iwowa monga zoticenjeza, ndipo zinalembedwa kuticenjeza ife, amene matsirizidwe a nthawi ya pansi pano adafika pa ife.

12 Cifukwa cace iyewakuyesa kuti ali ciriri, ayang'anire kuti angagwe,

13 Sicinakugwerani inu ciyeso koma ca umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi ciyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.

14 Cifukwa cace, okondedwa anga, thawani kupembedza mafano.

15 Ndinena monga kwa anzeru; lingirirani inu cimene ndinena.

16 Cikho ca dalitso cimene tidalitsa, siciri ciyanjano ca mwazi wa Kristu kodi? Mkate umene tinyema suli ciyanjano ca thupi la Kristu kodi?

17 Pakuti mkate ndiwo umodzi, cotero ife ambiri ndife thupi limodzi; pakuti ife tonse titengako ku mkate umodzi.

18 Tapenyani Israyeli monga mwa thupi; kodi iwo akudya nsembezo alibe ciyanjano ndi guwa la nsembe?

19 Ndinena ciani tsono? kuti coperekedwa nsembe kwa mafano ciri kanthu? Kapena kuti fane liri kanthu kodi?

20 Koma nditi kuti zimene amitundu apereka nsembe azipereka kwa ziwanda; ndipo sindifuna kuti inu muyanjane ndi ziwanda.

21 Simungathe kumwera cikho ca Ambuye, ndi cikho ca ziwanda; simungathe kulandirako ku gome la Ambuye, ndi ku gome la ziwanda.

22 Kapena kodi ticititsa nsanje Ambuye? Kodi mphamvu zathu ziposa iye?

23 Zinthu zonse ziloleka; koma sizipindula zonse. Zinthu zonse ziloleka; koma sizimanga zonse.

24 Munthu asafune zace za iye yekha, kama za mnzace.

25 Conse cogulitsidwa pa msika wa nyama, mudye, osafunsa kanthu cifukwa ca cikumbu mtima;

26 pakuti dziko lapansi liri la Ambuye, ndi kudzala kwace.

27 Ngati wina wa osakhulupira akuitanani, ndipo mufuna kupita; mudye comwe ciikidwa kwa inu, osafunsa kanthu, cifukwa ca cikumbu mtima.

28 Koma ngati wina akati kwa inu, Yoperekedwa nsembe iyi, musadye, cifukwa ca iyeyo wakuuza, ndi cifukwa ca cikumbu mtima.

29 Ndinena cikumbu mtima, si ca iwe mwini, koma ca winayo; 1 pakuti ufulu wanga uyesedwa ninji ndi cikumbu mtima ca wina?

30 Ngati ine ndilandirako mwacisomo, ndinenezedwa bwanji cifukwa ca ici cimene ndiyamikapo?

31 Cifukwa cace 2 mungakhale mudya, mungakhale mumwa, mungakhale mucita kanthu kena, citani zonse ku ulemerero wa Mulungu.

32 3 Khalani osakhumudwitsa, kapena Ayuda, kapena Ahelene, kapena Mpingo wa Mulungu;

33 monga 4 inenso ndikodweretsa onse m'zinthu zonse, wosafuna cipindulo canga, koma ca unyinjiwo, kuti apulumutsidwe.

11

1 Khalani onditsanza ine, monga inenso oditsanza Kristu.

2 Ndipo ndikutamandani kuti m'zinthu zonse mukumbukila ine, ndi kuti musunga miyambo monga ndinapereka kwa inu.

3 Koma ndifunakuti mudziwe, kuti mutu wa munthu yense ndiye Kristu; ndi mutu wa mkazi ndiye mwamuna; ndipo mutu wa Kristu ndiye Mulungu,

4 Mwamuna yense wobveka mutu, popemphera kapena ponenera, anyoza mutu wace.

5 Koma mkazi yense wakupemphera, kapena kunenera, wobvula mutu, anyoza mutu wace; pakuti kuli cimodzimodzi kumetedwa.

6 Pakuti ngati mkazi sapfunda, asengedwenso; koma ngati kusengedwa kapena kumetedwa kucititsa manyazi, apfunde,

7 Pakuti mwamuna sayenera kubvala pamutu, popeza akhala fanizo ndi ulemerero wa Mulungu: koma mkazi ali ulemerero wa mwamuna.

8 Pakuti mwamuna sakhala wa kwa mkazi; koma mkazi wa kwa mwamuna;

9 pakutinso mwamuna sanalengedwa cifukwa ca mkazi;

10 koma mkazi cifukwa ca mwamuna; cifukwa ca ici mkazi ayenera kukhala nao ulamuliro pamutu pace, cifukwa ca angelo.

11 Komanso mkazi sakhala wopanda mwamuna, kapena mwamuna wopanda mkazi, mwa Ambuye.

12 Pakuti monga mkazi aliwa kwa mwamuna, comweconso mwamuna ali mwa mkazi; koma zinthu zonse ziri za kwa Mu, lungu.

13 Lingirirani mwa inu nokha: Kodi nkuyenera kuti apemphere kwa Mulungu, wosapfunda mutu?

14 Kodi ubadwidwe womwe sutiphunzitsa kuti ngati mwamuna aweta tsitsi cimnyozetsa iye?

15 Koma ngati mkazi aweta tsitsi, kuli ulemerero kwa iye; pakuti tsitsi lace lapatsidwa kwa iye ngati cophimba.

16 Koma akaoneka wina ngati wotetana, tiribe makhalidwe otere, kapena ife, kapena Eklesia wa Mulungu.

17 Koma pakulalikira ici sinditama inu, popeza simusonkhanira cokoma, koma coipa.

18 Pakutitu poyamba posonkhana inu mu Mpingo, ndimva kuti pakhala malekano mwa inu; ndipo ndibvomereza penapo.

19 Pakuti kuyenera kuti pakhale mipatuko mwa inu, kuti iwo obvomerezedwa aonetsedwemwa inu.

20 Cifukwa cace, pakusonkhana inu pamodzi sikutheka kudya mgonero wa Ambuye;

21 pakuti pakudyaku yense athanga watenga mgonero wace wa yekha, ndipo wina ali ndi njala, ndi wina aledzera.

22 Nanga mulibe nyumba za kudyeramo ndi kumweramo? Kapena kodi munyoza Eklesia wa Mulungu, ndi kunyoza iwo amene alibe kanthu? Ndidzanena ciani kwa inu? Kodi ndidzatama inu m'menemo? Sindikutamani.

23 Pakuti ine ndinalandira kwa Ambuye, cimenenso ndinapereka kwainu, kuti Ambuye Yesu usikuuja anaperekedwa, anatenga mkate;

24 ndipo m'mene adayamika, ananyema, nati, ici ndi thupi langa la kwa inu; citani ici cikhale cikumbukilo canga.

25 Koteronso cikho, citatha cakudya, ndi kuti, Cikho ici ndi pangano latsopano m'mwazi wanga; citani ici, nthawi zonse mukamwa, cikhale cikumbukilo canga,

26 Pakuti nthawi zonse mukadya mkate uwu ndi kumwera cikho, mulalikira imfa ya Ambuye kufikira akadza iye.

27 Cifukwa cace yense amene akadyamkate, kapena akamwera cikho ca Ambuye kosayenera, adzakhala wocimwira thupi ndi mwazi wa Ambuye.

28 Koma munthu adziyese yekha, ndi kotero adye mkate, ndi kumwera cikho.

29 Pakuti iye wakudya ndi wakumwa, adya namwa ciweruziro kwa iye yekha, ngati sazindikira thupilo.

30 Cifukwa cace ambiri mwa inu afoka, nadwala, ndipo ambiri agona.

31 Koma ngati tikadadzizindikira tokha sitikadaweruzidwa.

32 Koma poweruzidwa, tilangidwa ndi Ambuye, kuti tingatsutsidwe pamodzi ndi dziko lapansi.

33 Cifukwa cace, abale anga, posonkhanira kudya, lindanani.

34 Ngati wina ali ndi njala adye-kwao; kuti mungasonkhanire kwa ciweruziro. Koma zotsalazo nelidzafotokoza pakudza ine.

12

1 Koma za mphatso zauzimu, abale, sindifuna kuti mukhale osadziwa.

2 Mudziwa kuti pamene munali amitundu, munatengedwa kunka kwa mafano aja osalankhula, monga munatsogozedwa.

3 Cifukwa cace ndikuuzani inu, kuti palibe munthu wakulankhula mwa Mzimu wa Mulungu, anena, Yesu ngwotembereredwa; ndipo palibe wina akhoza kunena, Yew ali Ambuye, koma mwa Mzimu Woyera.

4 Ndipo pali mphatso zosiyana, koma Mzimu yemweyo.

5 Ndipo pali mautumiki osiyana, koma Ambuye yemweyo.

6 Ndipo pali macitidwe osiyana, koma Mulungu yemweyo, wakucita zinthu zonse mwa onse.

7 Koma kwa yense kwapatsidwa maonekedwe a Mzimu kuti apindule nao.

8 Pakuti kwa mmodzi kwapatsidwa mwa Mzimu mau a nzeru; koma kwa mnzace mau a cidziwitso, monga mwa Mzimu yemweyo:

9 kwa wina cikhulupiriro, mwa Mzimu yemweyo; ndi kwa wina mphatso za maciritso, mwa Mzimu mmodziyo;

10 ndi kwa wina macitidwe a mphamvu; ndi kwa wina cinenero; ndi kwa wina cizindikiro ca mizimu; kwa wina malilime a mitundu mitundu; ndi kwa wina mamasulidwe a malilime.

11 Koma zonse izi acita Mzimu mmodzi yemweyo, nagawira yense payekha monga afuna.

12 Pakuti monga thupi liri limodzi, nilikhala nazo ziwalo zambiri; koma ziwalo zonse za thupilo, pokhala zambiri, ziri thupi limodzi; momwemonso Kristu.

13 Pakutinso mwa Mzimu mmodzi ife tonse rinabatizidwa kulowa m'thupi limodzi, ngakhale Ayuda, ngakhale Ahelene, ngakhale akapolo, ngakhale mfulu; ndipo tonse tinamwetsedwa Mzimu mmodzi.

14 Pakutinso thupisilikhala ciwalo cimodzi, koma zambiri.

15 Ngati phazi likati, Popeza sindiri dzanja, sindiri wa thupi; kodi siliri la thupi cifukwa ca ici?

16 Ndipo ngati khutu likati, Popeza sindiri diso, sindiri wa thupi; kodi siliri la thupi cifukwa ca ici?

17 Ngati thupi lonse likadakhala diso, kukadakhala kuti kununkhiza?

18 Koma tsopano, Mulungu anaika ziwalo zonsezo m'thupi, monga anafuna.

19 Koma ngati zonse zikadakhala ciwalo cimodzi, likadakhala kuti thupi?

20 Kama tsopano pali ziwalo zambiri, kama thupi limodzi.

21 Ndipo dise silingathe kunena kwa dzanja, Sindikufuna iwe, kapenanso mutu kwa mapazi, Sindikufunani inu.

22 Koma makamakatu ziwalozo zoyesedwa zofoka m'thupi, zifunika;

23 ndipo zimene tiziyesa Zocepa ulemum'thupi, pa izi tiika ulemu wocuruka woposa; ndi zinthu zosakoma zikhala naco cokometsera coposa,

24 Koma zokoma zathu ziribe kusowa; koma Mulungu analumikizitsa thupi, napatsa ulemu wocuruka kwa cosowaco; kuti kusakhale cisiyano m'thupi;

25 koma kuti ziwalo zifanane ndi kusamalana cinandicinzace,

26 Ndipocingakhale ciwalo cimodzi cimva cowawa, ziwalo zonse zimva pamodzi; cingakhale cimodzi cilemekezedwa, ziwalo zonse zikondwera naco pamodzi,

27 Koma inundinu thupi la Kristu, ndi ziwalo, yense pa yekha.

28 Ndipotu Mulunguanailea ena m'Eklesia, poyamba arumwi, aciwiri aneneri, acitatu aphunzitsi, pamenepo zozizwa, pomwepo mphatso zamaciritso, mathandizo, maweruziro, malilime a mitundu mitundu.

29 Kodi ali onse atumwi? Ali aneneri onse kodi? Ali aphunzitsi onse? Ali onse ocita zozizwa?

30 Ali nazo mphatso za maciritso onse kodi? Kodi onse alankhula ndi malilime? Kodi onse amasulira mau?

31 Koma funitsitsani mphatso zoposa. Ndipo ndikuonetsani njira yokoma yoposatu.

13

1 Ndingakhale ndilankhula malilime a anthu, ndi a angelo, koma ndiribe cikondi, ndikhala mkuwa woomba, kapena nguli yolira.

2 Ndipo ndingakhale ndikhoza kunenera, ndipo ndingadziwe zinsinsi zonse, ndi nzeru zonse, ndipo ndingakhale ndiri naco cikhulupiriro conse, kuti ndikasendeza mapiri, koma ndiribe cikondi, ndiri cabe.

3 Ndipo ndingakhale ndipereka cuma cangaconsekudyetsa osauka, ndipo ndingakhalendipereka thupi langa alitenthe m'moto, koma ndiribe cikondi, sindipindula kanthu ai.

4 Cikondi cikhala cilezere, ciri cokoma mtima; cikondi sicidukidwa; cikondi sicidziwa kudzitamanda, sicidzikuza,

5 sicicita zosayenera, sicitsata za mwini yekha, sicipsa mtima, sicilingirira zoipa;

6 sicikondwera ndi cinyengo, koma cikondwera ndi coonadi;

7 cikwirira zinthu zonse, cfkhulupirira zinthu zonse, ciyembekeza zinthu zonse, cipirira zinthu zonse.

8 Cikondi sicitha nthawizonse, koma kapena zonenera zidzakhala cabe, kapena malilime adzaleka, kapena nzeru idzakhala cabe.

9 Pakuti ife tidziwa mderamdera, ndimo tinenera mderamdera.

10 Koma pamene cangwiro cafika, tsono camderamdera cidzakhalacabe.

11 Pamene ndinali mwana, ndinalankhula ngati mwana, ndinalingirira ngati mwana, ndinawerenga ngati mwana; tsopano ndakhala munthu, ndayesa cabe zacibwana.

12 Pakuti tsopano tipenya m'kalirole, ngati cimbuuzi; koma R pomwepo maso ndi maso. Tsopano ndizindikira mderamdera; koma pomwepo ndidzazindikiratu, monganso ndazindikiridwa.

13 Ndipo tsopano zitsala cikhulupiriro, dyembekezo, cikondi, zitatu izi; koma cacikuru ca izi ndico cikondi.

14

1 Tsatani cikondi; koma funitsitsani mphatsozauzimu, koma koposa kuti mukanenere.

2 Pakuti iye wakulankhula lilime salankhula ndi anthu, koma ndi Mulungu; pakuti palibemunthu akumva; koma mumzimu alankhula zinsinsi.

3 Koma iye wakunenera alankhula ndi anthu comangirira ndi colimbikitsa, ndi cosangalatsa,

4 Iye wakulankhula lilime, adzimangirira yekha, koma iye wakunenera amangirira Mpingo.

5 Ndipo ndifuna inu nonse mula'nkhule malilime, koma makamaka kuti mukanenere; ndipo wakunenera aposa wakulankhula malilime, akapanda kumasulira, kuti Mpingo ukalandire comangirira.

6 Koma tsopano, abale, ngati ndidza kwa inu ndi kulankhula malilime, ndikaku, pindulitsani ciani, ngati sindilankhui landi inu kapena m'bvumbulutso, kapena m'cidziwitso, kapena m'cinenero, kapena m'ciphunzitsot

7 Ngakhale zinthu zopanda moyo, zopereka mau, ngati toliro, kapena ngoli, ngati sizisiyanitsa maliridwe, cidzazindikirikabwanji cimene ciombedwa kapena kuyimbidwa?

8 Pakuti ngad Lipenga lipereka mao osazindikirika, adzadzikonzera ndani kunkhondo?

9 Momwemonso inu ngati mwa lilime simupereka mau omveka bwino, kudzazindikirika bwanji cimene cilankhulidwa? Pakuti mudzakhala olankhula kumlengalenga.

10 Iripo, kaya, mitundu yambiri yotere ya mau pa dziko lapansi, ndipo palibe kanthu kasowa mau.

11 Cifukwa cace, ngati sindidziwa mphamvu ya mauwo ndidzakhala kwa iye wolankhulayo wakunja, ndipo wolankhulayo adzakhala wakunja kwaine.

12 Momwemo inunso, popeza muli ofunits its a mphatso zauzimu, funani kuti mukacuruke kukumangirira kwa Mpingo,

13 Cifukwa cace wolankhula lilime, apemphere kuti amasule.

14 Pakuti ngati ndipemphera m'lilime, mzimu wanga upemphera, koma cidziwitso canga cikhala cosabala kanthu.

15 Kuli ciani tsono? Ndidzapemphera ndi mzimu, koma ndidzapempheranso ndi cidziwitso canga; ndidzayimba ndi mzimu, koma ndidzayimbanso ndi cidziwitso.

16 Cifukwa ngati udalitsa ndi mzimu, nanga iye wakukhala wosaphunzira adzati Amen bwanji, pa kuyamika kwako, popeza sadziwa cimene unena?

17 Pakutitu iwe uyamika bwino, koma winayo samangiriridwa.

18 Ndiyanillca Mulungu kuti ndilankhula malilime koposa inu nonse;

19 koma mu Mpingo ndifuna kulankhula mau asanu ndi cidziwitso canga, kutinso ndikalangize ena, koposa kulankhula mau zikwi m'lilime.

20 Abale, musakhale ana m'cidziwitso, koma m'coipa khalani makanda, koma m'cidziwitso akulu misinkhu.

21 Kwalembedwa m'cilamulo, Ndi anthu amalilime ena ndipo ndi milomo yina ndidzalankhula nao anthu awa; ndipo kungakhale kutero sadzamva Ine, anena Ambuye.

22 Cotero malilime akhala ngati cizindikilo, si kwa iwo akukhulupira, koma kwa iwo osakhulupira; koma kunenera sikuli kwa iwo osakhulupira, koma kwa two amene akhulupira.

23 Cifukwa cace, ngati Mpingo wonse akasonkhane pamodzi, ndi onse akalankhule malilime, ndipo akalowemo anthu osaphunzira kapena osakhulupira, kodi sadzanena kuti mwayaruka?

24 Koma ngati onse anenera, ndipo alowamo wina wosakhulupirira kapena wosaphunzira, atsutsidwa ndi onse; aweruzidwa ndi onse;

25 zobisika za mtima wace zionetsedwa; ndipo cotero adzagwa nkhope yace pansi, nadzagwadira Mulungu, nadzalalikira kuti Mulungu ali ndithu mwa inu.

26 Nanga ciani tsono, abale? Pamene musonkhana, yense ali nalo salmo, ali naco ciphunzitso, ali nalo bvumbulutso, ali nalo lilime, ali naco cimasuliro. Mucite zonse kukumangirira.

27 Ngati wina alankhula lilime, acite ndi awiri, koma oposa atatu iai, ndipo motsatana; ndipo mmodzi amasulire.

28 Koma ngati palibe womasulira, akhale cete mu Mpingo, koma alankhule ndi iye yekha, ndi Mulungu.

29 Ndipo aneneri alankhule awiri kapena atatu, ndi ena azindikire.

30 Koma ngati kanthu kabvumbulutsidwa kwa wina wakukhalapo, akhale cete woyambayo.

31 Pakuti mukhoza nonse kunenera mmodzi mmodzi, kuti onse aphunzire, ndi onse afulumidwe;

32 ndipo mizimu ya aneneri imvera aneneri;

33 pakuti Mulungu sali Mulungu wa cisokonezo koma wa mtendere; monga mwa Mipingo yonse ya oyera mtima.

34 Akazi akhale cete m'Mipingo. Pakuti vsikuloledwa kwa iwo kulankhula, Koma akhale omvera, mongansocilamulo cmena,

35 Koma ngati afuna kuphunzirakanthu afunseamuna ao aiwo okha kwao; pakuti kunyazitsa mkazi kulankhula mu Mpingo.

36 Kodi mau a Mulungu anatutuka kwa iw? kapena anafika kwa inu nokha?

37 Ngatiwinaayesa kuti ali mneneri, kapena wauzimu; azindikire kuti zimene ndilemba kwa inu ziri lamulo la Ambuye,

38 Koma ngati wina akhale wosadziwa, akhale wosadziwa.

39 Cifukwa cace; abale anga, funitsitsani kunenera, ndipo musaletse kulankhula malilime.

40 Koma zonse zicitike koyenera ndi kolongosoka.

15

1 Ndipo ndikudziwitsani, abale, Uthenga Wabwino umene ndinakulalikirani inu, umenenso munalandira, umenenso muimamo,

2 umenenso mupulumutsidwa nao ngati muugwiritsa monga momwe ndinalalikira kwa inu; ngati simunakhulupira cabe.

3 Pakuti ndinapereka kwa inu poyamba, cimenenso ndinalandira, kuti Kristuanafera zoipa zathu, mongamwa malembo;

4 ndi kuti anaikidwa; ndi kutianaukitsidwa tsiku lacitatu, monga mwa malembo;

5 ndi kuti anaonekera kwa Kefa; pamenepo kwa khumi ndi awiriwo;

6 pomwepo anaoneka pa nthawi imodzi kwa abale oposa mazana asanu, amene ocuruka a iwo akhala kufikira tsopano, koma ena agona;

7 pomwepoanaonekera kwa Yakobo; pamenepo kwa: atumwi onse;

8 ndipo potsiriza pace pa onse, anaoneka kwa inenso monga mtayo.

9 Pakuti ine ndiri wamng'ono wa atumwi, ndine wosayenera kuchedwa mtumwi, popeza ndinalondalonda Eklesia wa Mulungu.

10 Koma ndi cisomo ca Mulungu ndiri ine amene ndiri; ndipo cisomo cace ca kwa ine sicinakhala copanda pace, koma ndinagwirira nchito yocuruka ya iwo onse; koma si ine, komacisomo ca Mulungu cakukhala ndi ine.

11 Ngati ine tsono, kapena iwowa, kotero tilalikira, ndi kotero munakhulupira.

12 Koma ngati Kristu alalikidwa kuti waukitsidwa kwa akufa, nanga ena mwa inu anena bwanjikuti kulibe kuuka kwa akufa?

13 Koma ngati kulibe kuuka kwa akufa, Kristunso sanaukitsidwa;

14 ndipo ngati Kristu sanaukitsidwakulalikira kwathu kuli cabe, cikhulupiriro canunso ciri cabe.

15 Ndiponso ife tipezedwa mboni zonama za Mulungu; cifukwa n tinacita umboni kunena za Mulungu kuti anaukitsa Kristu; amene sanamuukitsa, ngati kuli tero kuti akufa saukitsidwa,

16 Pakuti ngati akufa saukitsidwa, Kristunso sanaukitsidwa;

17 ndipo ngati Kristu sanaukitsidwa, cikhulupiriro canu ciri copanda pace; muli cikhalire m'macimo anu.

18 Cifukwa cace iwonso akugona mwa Kristu anatayika.

19 Ngati tiyembekezera Kristu m'moyo uno wokha, tiri ife aumphawi oposa a anthu onse,

20 Koma tsopano Kristu waukitsidwa kwa akufa, cipatso coundukula ca iwo akugona.

21 Pakuti monga imfa inadza mwa munthu, kuuka kwa akufa kunadzanso mwa munthu.

22 Pakuti mongamwa Adamu onse amwalira, coteronso mwa Kristu onse akhalitsidwa ndi moyo.

23 Koma yense m'dongosolo lace la iye yekha, cipatso coundukula Kristu, pomwepo iwo a Kristu, pa kubwera kwace.

24 Pomwepo pali cimariziro, pamene adzapereka ufumu kwa Mulungu, ndiye Atate, atatha kuthera ciweruzo conse, ndi ulamuliro wonse, ndi mphamvu yomwe.

25 Pakuti ayenera kucita ufumu kufikira ataika adani onse pansi pa mapazi ace.

26 Mdani wotsiriza amene adzathedwa ndiye imfa.

27 Pakuti Iye anagonjetsa zonse pansi pa mapazi ace. Koma pamene anena kutizonse zagonjetsedwa, kuzindikirika kuti sawerengapo Iye amene anagonjetsa zonsezo kwa Iye.

28 Ndipo pamene zonsezo: zagonjetsedwa kwa iye, pomwepo Mwana yemwe adzagonjetsedwa kwa iye amene anamgonjetsera zinthuzonse; kuti Mulungu akhale zonse mu zonse.

29 Ngati si kutero, adzacita ciani iwo amene abatizidwa cifukwa ca akufa? Ngatiakufa saukitsidwa konse, abatizidwa cifukwa ninji cifukwa ca iwo?

30 Nanga 1 ifenso tiri m'moopsya bwanji nthawi zonse?

31 2 Ndifa tsiku ndi tsiku, ndilumbira pa kudzitamandira kwa inu, abale, kumene ndiri nako mwa Kristu Yesu, Ambuye wathu.

32 3 Ngati odinalimbana ndi zirombo ku Efeso monga mwa munthu, ndipindulanji? Ngati akufa saukitsidwa, 4 tidye timwepakuti mawa timwalira.

33 Musanyengedwe; 5 mayanjano oipa aipsa makhalidwe okoma

34 6 Ukani molungama, ndipo musacimwe; pakuti enaalibe cidziwitso ca Mulungu, Ndilankhula kunyaza inu.

35 Koma wina adzati, 7 Akufa aukitsidwa bwanji? Ndipo adza nalorhupi lotani?

36 Wopusa iwe, 8 cimene ucifesa wekha sieikhalitsi'dwanso camoyo, ngati sicifa;

37 ndipo cimene ufesa, sufesa thupi limene lidzakhala, koma mbeu yokhakapenaya tirigu kapena ya, mtundu wina;

38 koma Mulungu iaipatsa thupi mongaafuna; ndi, kwa mbeu yonse thupi lace lace.

39 Nyama yonse siiri imodzimodzi; koma yinandi Ya anthu, ndi yina ndiyo nyama ya zoweta, ndi yina ndiyo nyama ya mbalame, ndi yina ya nsomba.

40 Palinso matupi am'mwamba, ndi matupi apadziko: koma ulemerero wa lam'mwamba ndi wina, ndi ulemerero wa lapadziko ndi winanso.

41 Kuli ulemerero wa dzuwa, ndi ulemerero wina wa mwezi, ndi ulemerero wina wa nyenyezi; pakuti nyenyezi isiyana ndi nyenyezi m'ulemerero.

42 9 Comweconso kudzakhala kuuka kwa akufa. Lifesedwa m'cibvundi, liukitsidwa m'cisabvundi;

43 10 lifesedwa m'mnyozo, liukitsidwa m'ulemerero; lifesedwa m'cifoko, liukitsidwa mumphamvu;

44 lifesedwa thupi Iacibadwidwe, liukitsidwa thupi lauzimu. Ngati pali thupi Iacibadwidwe, palinso lauzimu.

45 Koteronso kwalembedwa, 11 Munthu woyamba, Adamu, anakhala mzimu wamoyo. 12 Adamu wotsirizayo anakhala mzimu wakulenga moyo.

46 Koma cauzimu siciri coyamba, koma cacibadwidwe; pamenepo cauzimu.

47 13 Munthu woyambayo ali wapansi, wanthaka. Munthu waciwiri ali wakumwamba.

48 14 Monga wanthakayo, ateronso anthaka; ndi monga wakumwamba, ateronso akumwamba.

49 Ndipo 15 monga tabvaia fanizo la wanthakayo, tidzabvalanso fanizo la wakumwambayo.

50 Koma ndinena ici, abale, kuti 16 thupi ndi mwazi sizingathe kulowa Ufumu wa Mulungu; kapena cibvundi sicilowa cisabvundi.

51 Taonani, ndikuuzani cinsinsi; 17 sitidzagona tonse, koma tonse tidzasandulika,

52 m'kamphindi, m'kutwanima kwa diso, pa lipenga lotsiriza; pakuti 18 lipenga lidzalira, ndipo akufa adzaukitsidwa osabvunda, ndipoife tidzasandulika.

53 Pakuti cobvunda ici ciyenera kubvala cisabvundi, ndi 19 caimfa ici kubvala cosafa.

54 Ndipo pamene cobvunda ici cikadzabvala cisabvundi ndi caimfa ici cikadzabvala cosafa, pamenepo padzacitika mau olembedwa, 20 Imfayo yamezedwa m'cigonjetso.

55 21 Imfawe, cigonjetso cako ciri kuti? Imfawe, mbola yako iri kuti?

56 Koma mbola ya imfa ndiyo ucimo; koma 22 mphamvu ya ucimo ndiyo cilamulo:

57 koma 23 ayamikike Mulungu, amene atipatsa ife cigonjetso mwa Ambuye wathu Yesu Kristu.

58 Cifukwa cace, abale anga okondedwa, 24 khalani okhazikika, osasunthika, akucuruka mu ncbitoya Ambuye, nthawi zonse, podziwa kuti kucititsa kwanu sikuli cabe mwa Ambuye.

16

1 Koma za copereka ca kwa oyera mtima, mongandinalangiza Mipingo ya ku Galatiya, motero citani inunso.

2 Tsiku loyamba la sabata yense wa inu asunge yekha; monga momwe anapindula, kuti zopereka zisacitike pakudza ine.

3 Ndipo pamene ndifika, ndidzatuma iwo amene mudzawayesa oyenera, ndi akalata, apite nayo mphatso yanu ku Yerusalemu.

4 Ndipo ngati kuyenera kwa ine kupitanso, adzapita nane.

5 Koma ndidzadza kwa inu, nditapyola Makedoniya; pakuti ndidzapyola Makedoniya;

6 ndipo kapena ndidzakhalitsa ndi inu, kapenanso kugonera nyengo yacisanu kuti mukandiperekeze ine kumene kuli konse ndipitako,

7 Pakuti sindifuna kukuonani tsopano popitirira; pakuti ndiyembekeza kukhala ndi inu nthawi, ngati alola Ambuye.

8 Koma ndidzakhaia ku Efeso kufikira Penteskoste,

9 Pakuti panditsegukira pa khomo lalikuru ndi locititsa, ndipo oletsana nafe ndi ambiri.

10 Koma akadza Timoteo, penyani kuti akhale ndi inu wopanda mantha; pakuti agwira nchito ya Ambuye, monganso ine;

11 cifukwa cace munthu asampeputse, Koma mumperekeze mumtendere, kuti akadze: kwa ine; pakuti ndimuyembekezera pamodzi ndi abale,

12 Koma za Apolo, mbaleyo, ndamuumiriza iye, adze kwa inu pamodzi ndi abale; ndipo sicinali cifuniro cace kuti adze tsopano, koma adzafika pameneaona nthawi.

13 Dikirani, cirimikani m'cikhulupiriro; dzikhalitseni amuna, limbikani.

14 Zanu zonse zicitike m'cikondi.

15 Koma ndikupemphani inu, abale, (mudziwa banja la Stefana, kuti ali cipatsocoundukula ca Akaya, ndi kuti anadziika okha kutumikira oyera mtima),

16 kuti inunso mubvomere otere, ndi yense wakucita nao, ndi kugwiritsa nchito.

17 Koma ndikondwera pa kudza kwao kwa Stefana, ndi Fortunato, ndi Akayiko; cifukwa iwo anandikwaniritsa cotsalira canu.

18 Pakuti anatsitsimutsa mzimu wanga ndi wanu; cifukwa cace muzindikire otere.

19 Mipingo ya ku Asiya ilankhula inu. Akulankhulani ndithu inu mwa Ambuye, Akula ndi Priska, pamodzi ndi Mpingo wa m'nyumba yao,

20 Akulankhulani inu abale onse. Lankhulanani ndi kupsompsona kopatulika.

21 Kulankhula kwa ine Paulo ndi dzanja langa.

22 Ngati wina sakonda Ambuye, akhale wotembereredwa. Akudza Ambuye.

23 Cisomo ca Ambuye Yesu Kristu cikhale ndi inu.

24 Cikondi canga cikhale ndi inu nonse mwa Kristu Yesu. Amen.