1 PAULO ndi Timoteo, akapolo a Yesu Kristu, kwa oyera mtima onse mwa Kristu Yesu, akukhala ku Filipi, pamodzi ndi oyang'anira ndi atumiki:
2 Cisomo kwa inu ndi mtendere za kwa Mulungu Atate wathu ndi Ambuye Yesu Kristu.
3 Ndiyamika Mulungu wanga pokumbukira inu ponse;
4 nthawi zonse m'pembedzero langa lonse la kwa inu nonse ndicita pembedzerolo ndi kukondwera,
5 cifukwa ca ciyanjano canu cakuthandizira Uthenga Wabwino, kuyambira tsiku loyambalo, kufikira tsopano lino;
6 pokhulupira pamenepo, kuti iye amene anayamba mwa inu nchito yabwino, adzaitsiriza kufikira tsiku la Yesu Kristu;
7 monga kundiyenera ine kuyesa za inu nonse, popeza ndiri nako m'mtima mwanga, kuti inu m'zomangira zanga, ndipo m'codzikanira, ndi matsimikizidwe a Uthenga Wabwino, inu nonse muli oyanjana nane m'cisomo.
8 Pakuti Mulungu ali mboni yanga, kuti ndilakalaka inu nonse m'phamphu la mwa Kristu Yesu.
9 Ndipo ici ndipempha, kuti cikondi canu cisefukire cionjezere, m'cidziwitso, ndi kuzindikira konse;
10 kuti mukayese inu zinthu zosiyana; kuti mukakhale a mtima woona ndi wosalakwa, kufikira tsiku la Kristu;
11 odzala nacocipatso ca cilungamo cimene ciri mwa Yesu Kristu, kucitira Mulungu ulemerero ndi ciyamiko.
12 Koma abale, ndifuna kuti muzindikire kuti zija za kwa ine zidacita makamaka kuthandizira Uthenga Wabwino;
13 kotero kuti zomangira zanga zinaonekera mwa Kristu m'bwalo lonse da alonda, ndi kwa onse ena;
14 ndi kuti unyinji wa abale mwa Ambuye, pokhulupirira m'zomangira zanga, alimbika mtima koposa kulankhula mau a Mulungu opanda mantha.
15 Enatu alalikiranso Kristu cifukwa ca kaduka ndi ndeu; koma enanso cifukwa ca kukoma mtima;
16 ena atero ndi cikondi, podziwa kuti anandiika ndicite eokanira ca Uthenga Wabwino;
17 koma ena alalikira Kristu mocokera m'cotetana, kosati koona, akuyesa kuti adzandibukitsira cisautso m'zomangira zanga.
18 Potero nciani? Cokhaco kuti monsemo, ngati pamaso pokha, ngati m'coonadi, Kristu alalikidwa; ndipo m'menemo ndikondwera, komanso ndidzakondwera.
19 Pakuti ndidziwa kuti ici cidzandicitira ine cipulumutso, mwa pembedzero lanu ndi mwa kundipatsako kwa Mzimu wa Yesu Kristu;
20 monga mwa kulingiriritsa ndi ciyembekezo canga, kuti palibe cinthu cidzandicititsa manyazi, komatu mwa kulimbika mtima konse, monga nthawi yonse, tsopanonso Kristu adzakuzidwa m'thupi langa, kapena mwamoyo, kapena mwa imfa.
21 Pakuti kwa ine kukhala ndi moyo ndiko Kristu, ndi kufa kuli kupindula.
22 Koma ngati kukhala ndi moyo m'thupi, ndiko cipatso ca nchito yanga, sindizindikiranso cimene ndidzasankha.
23 Koma ndipanidwa nazo ziwirizi, pokhala naco colakalaka ca kucoka kukhala ndi Kristu, ndiko kwabwino koposa-posatu;
24 koma kukhalabe m'thupi ndiko kufunika koposa, cifukwa ca inu.
25 Ndipo pokhulupirira pamenepo ndidziwa kuti ndidzakhala, ndi kukhalitsa ndi inu nonse, kuonjezeracimwemwe ca cikhulupiriro canu;
26 kuti kudzitamandira kwanu kucuruke m'Kristu Yesu mwa ine, mwa kukhalanso ine kwa inu.
27 Cokhaci, mayendedwe anu ayenere Uthenga Wabwino wa Kristu: kuti, ndingakhale nditi ndirinkudza ndi kuona inu, ndingakhale nditi ndiri kwina, ndikamva za kwa inu, kuti mucirimika mu mzimu umodzi, ndi kugwirira pamodzi ndi moyo umodzi cikhulupiriro ca Uthenga Wabwino;
28 osaopa adani m'kanthu konse, cimene ciri kwa iwowa cisonyezo ca cionongeko, koma kwa inu ca cipulumutso, ndico ca kwa Mulungu;
29 kuti kwapatsidwa kwa inu kwaufulu cifukwa ca Kristu, si kukhulupirira kwa iye kokha, komatunso kumva zowawa cifukwa ca iye,
30 ndi kukhala naco inu cilimbano comweci mudaciona mwa ine, nimukumva tsopano ciri mwa ine.
1 Ngati tsono muli citonthozo mwa Kristu, ngati cikhazikitso ca cikondi, ngati ciyanjano ca Mzimu, ngati phamphu, ndi zisoni,
2 kwaniritsani cimwemwe canga, kuti mukalingalire mtima zomwezo, akukhala naco cikondi comwe, a moyo umodzi, olingalira mtima umodzi;
3 musacite kanthu monga mwa cotetana, kapena monga mwa ulemerero wopanda pace, komatu ndi kudzicepetsa mtima, yense ayese anzace omposa iye mwini;
4 munthu yense asapenyerere zace za iye yekha, koma yense apenyererenso za mnzaceo
5 Mukhale nao mtima m'kati mwanu umene unalinso mwa Kristu Yesu,
6 ameneyo, pokhala nao maonekedwe a Mulungu, sanaciyesa colanda kukhala wofana ndi Mulungu,
7 koma anadzikhuthula yekha, natenga maonekedwe akapolo, nakhala m'mafanizidwe a anthu;
8 ndipo popezedwa m'maonekedwe ngati munthu, anadzicepetsa yekha, nakhala womvera kufikira imfa, ndiyo imfa ya pamtanda.
9 Mwa icinso Mulungu anamkwezetsa iye, nampatsa dzina limene liposa maina onse,
10 kuti m'dzina la Yesu bondo liri lonse lipinde, la za m'mwamba ndi za padziko, ndi za pansi pa dziko,
11 ndi malilime onse abvomere kuti Yesu Kristu ali Ambuye, kucitira ulemu Mulungu Atate.
12 Potero, okondedwa anga, monga momwe mumvera nthawi zonse, posati pokha pokha pokhala ine ndiripo, komatu makamaka tsopano pokhala ine palibe, gwirani nchito yace ya cipulumutso canu ndi mantha, ndi kunthunthumira;
13 pakuti wakucita mwa inu kufuna ndi kucita komwe, cifukwa ca kukoma mtima kwace, ndiye Mulungu,
14 Citani zonse kopanda madandaulo ndi makani,
15 kuti mukakhale osalakwa ndi oona, ana a Mulungu opanda cirema pakati pa mbadwo wokhotakhota ndi wopotoka, mwa iwo amene muonekera monga mauniko m'dziko lapansi,
16 akuonetsera mau a movo; kuti ine ndikakhale wakudzitamandira: nao m'tsiku la Kristu, kuti sindinathamanga cabe, kapena kugwiritsa nchito cabe.
17 Komatu ngatinso ndithiridwa pa nsembe ndi kutumikira kwa cikhulupiriro canu, ndikondwera, ndipo ndikondwera pamodzi ndi inu nonse;
18 momwemonso kondwerani inu, nimukondwere pamodzi ndi ine.
19 Koma ndiyembekeza mwa Ambuye Yesu kuti ndidzatumiza Timoteo kwa inu msanga, kuti inenso nditonthozeke bwino pozindikira za kwa inu.
20 Pakuti ndiribe wina wa mtima womwewo, amene adza: samalira za kwa inu ndi mtima woona.
21 Pakuti onsewa atsata za iwo okha, si za Yesu Kristu.
22 Koma muzindikira matsimikizidwe ace, kuti, monga mwana acitira atate wace, anatumikira pamodzi ndi ine Uthenga Wabwino.
23 Ameneyo ndithu tsono ndiyembekeza kumtuma posacedwa m'mene ndikapenyerera za kwa ine zidzatani;
24 koma ndikhulupirira mwa Ambuye kuti ine ndekhanso ndidzadza msanga.
25 Koma ndinayesa nkufunika kutuma kwa inu Epafrodito mbaleyo, ndiye wanchito mnzanga ndi msilikari mnzanga, ndiye mtumwi wanu, ndi wonditumikira pa cosowa canga;
26 popeza anali wolakalaka inu nonse, nabvutika mtima cifukwa mudamva kuti anadwala.
27 Pakutinso anadwaladi pafupi imfa; komatu Mulungu anamcitira cifundo; koma si iye yekha, komatu inenso, kuti ndisakhale naco cisoni cionjezere-onjezere.
28 Cifukwa cace ndamtuma iye cifulumizire, kuti pakumuona mukakondwerenso, ndi inenso cindicepere cisoni.
29 Cifukwa cace mumlandire mwa Ambuye, ndi cimwemweconse; nimucitire ulemu oterewa;
30 pakuti cifukwa lea nchito ya Kristu anafikira pafupi imfa, wosasamalira moyo wace, kuti z akakwaniritse ciperewero ca utumiki wanu wa kwa ine.
1 Cotsalira, abale anga, kondwerani mwa Ambuye. Kulembera zomwezo kwa inu, sikundibvuta ine, koma kwa inu kuli kukhazikitsa.
2 Penyererani agaru, penyererani ocita zoipa, penyererani coduladula;
3 pakuti ife ndife mdulidwe, akutumikira popembedza ndi Mzimu wa Mulungu, nadzitamandira mwa Yesu Kristu, osakhulupirira m'thupi;
4 ndingakhale inenso ndiri nako kakukhulupirira m'thupi; ngati wina yense ayesa kukhulupirira m'thupi, makamaka ineyu;
5 wodulidwa tsiku lacisanu ndi citatu, wa mbadwo wa Israyeli, wa pfuko la Benjamini, Mhebri wa mwa Ahebri; monga mwa lamulo, Mfarisi;
6 monga mwa cangu, wolondalonda Eklesia; monga mwa cilungamo ca m'lamulo wokhala wosalakwa ine.
7 Komatu zonse zimene zinandipindulira, zomwezo ndinaziyesa citayiko cifukwa ca Kristu.
8 Komatu zeni zeninso ndiyesa zonse zikhale citayiko cifukwa ca mapambanidwe a cizindikiritso ca Kristu Yesu Ambuye wanga, cifukwa ca Iyeyu ndinatayikitsa zinthu zonse, ndipo ndiziyesa zapadzala, kuti ndikadzionjezere Kristu,
9 ndi kupezedwa mwa iye, wosati wakukhala naco cilungamo canga ca m'lamulo, koma cimene ca mwa cikhulupiriro ca Kristu, cilungamoco cocokera mwa Mulungu ndi cikhulupiriro;
10 kuti ndimzindikire iye, ndi mphamvu ya kuuka kwace, ndi ciyanjano ca zowawa zace, pofanizidwa ndi imfa yace;
11 ngati nkotheka ndikafikire kuuka kwa akufa.
12 Si kunena kuti ndinalandira kale, kapena kuti ndatha kukonzeka wamphumphu; koma ndilondetsa, ngatinso ndikacigwire ici cimene anandigwirira Yesu Kristu.
13 Abale, ine sindiwerengera ndekha kuti ndatha kucigwira: koma cinthu cimodzi ndicicita; poiwaladi zam'mbuyo, ndi kutambalitsira zam'tsogolo,
14 ndilondetsa polekezerapo, kutsatira mfupo wa maitanidwe akumwamba a Mulungu a mwa Kristu Yesu.
15 Tonsefe amene tsono tidakonzeka amphumphu, tilingirire ici mumtima; ndipo ngati kuli kanthu mulingirira nako kwina mumtima, akanso Mulungu adzabvumbulutsira inu;
16 cokhaci, kumene tidafikirako, mayendedwe athu alinganeko.
17 Abale khalani pamodzi akutsanza anga, ndipo yang'anirani iwo akuyenda kotero monga muli ndi ife citsanzo canu.
18 Pakuti ambiri amayenda, za amene ndinakuuzani kawiri kawiri, ndipo tsopanonso ndikuuzani ndi kulira, ali adani a mtanda wa Kristu;
19 citsiriziro cao ndico kuonongeka, mulungu wao ndiyo niimba yao, ulemerero wao uli m'manyazi ao, amenealingirira za padziko.
20 Pakuti ufulu wathu uli Kumwamba; z kucokera komwenso tilindirira Mpulumutsi, Ambuye Yesu Kristu;
21 amene adzasanduliza thupi lathu lopepulidwa, lifanane nalo thupi lace la ulemerero, monga mwa macitidwe amene akhoza kudzigonjetsera nao zinthu zonse.
1 Potero, abale anga okondedwa, olakalakidwa, ndinu cimwemwe canga ndikorona wanga, cirimikani motere mwa Ambuye, okondedwa.
2 Ndidandaulira Euodiya, ndidandaulira Suntuke, alingirire ndi mtima umodzi mwa Ambuye.
3 Inde, ndikupemphaninso, mnzanga wa m'goli woona, muthandize akazi awa amene anakangalika nane pamodzi mu Uthenga Wabwino, pamodzi ndi Klementonso, ndi otsala aja anchito anzanga, amene maina ao ali m'buku la moyo.
4 Kondwerani mwa Ambuye nthawi zonse: ndibwerezanso kutero, kondwerani.
5 Kufatsa kwanu kuzindikirike ndi anthu onse. Ambuye ali pafupi.
6 Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi ciyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu.
7 Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana cidziwitso conse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Kristu Yesu.
8 Cotsalira, abale, zinthu ziri zonse zoona, ziri zonse zolemekezeka, ziri zonse zolungama, ziri zonse zoyera, ziri zonse zokongola, ziri zonse zimveka zokoma; ngati kuli cokoma mtima cina, kapena citamando cina, zilingirireni izi.
9 Zimenenso mudaziphunzira, ndi kuzilandira, ndi kuzimva, ndi kuziona mwa ine, zomwezo citani; ndipo Mulungu wa mtendere adzakhala pamodzi ndi inu.
10 Koma ndinakondwera mwa Ambuye kwakukuru, kuti tsopano munatsitsimukanso kulingirira mtima za kwa ine, kumenekonso munalingirirako, koma munasowa pocitapo.
11 Si kuti ndinena monga mwa ciperewero, pakuti ndaphunzira ine, kuti zindikwanire ziri zonse ndiri nazo.
12 Ndadziwa ngakhale kupeputsidwa, ndadziwanso kusefukira; konseko ndi m'zinthu zonse ndalowa mwambo wakukhuta, ndiponso wakumva njala; wakusefukira, ndiponso wakusowa.
13 Ndikhoza zonse mwa iye wondipatsa mphamvuyo.
14 Koma munacita bwino kuti munayanjana nane m'cisautso canga.
15 Koma mudziwanso inu nokha, inu Afilipi, kuti m'ciyambi ca Uthenga Wabwino, pamene ndinacoka kuturuka m'Makedoniya, sunayanjana nane Mpingo umodzi wonse m'makhalidwe a copereka ndi colandira; koma inu nokha;
16 pakuti m'Tesalonikanso munanditumizira pa cosowa canga kamodzi kapena kawiri.
17 Sikunena kuti nditsata coperekaco, komatu nditsata cipatsocakucurukira ku ciwerengero canu.
18 Koma ndiri nazo zonse, ndipo ndisefukira; ndadzazidwa, popeza ndalandira kwa Epafrodito zija zidacokera kwanu, mnunkho wa pfungo labwino, nsembe yolandirika, yokondweretsa Mulungu.
19 Koma Mulungu wanga adzakwaniritsa cosowa canu ciri conse monga mwa cuma cace m'ulemerero mwa Kristu Yesu.
20 Ndipo kwa Mulungu ndi Atate wathu kukhale ulemerero ku nthawi za nthawi, Amen.
21 Lankhulani woyera mtima ali yense mwa Kristu Yesu. Abalewo akukhala ndiine alankhula inu.
22 Oyera mtima onse alankhula inu, koma makamaka-fwo a banja la Kaisara.
23 Cisomo ca Ambuye Yesu Kristu cikhale ndi mzimu wanu.