1 PAULO, ndi Silvano, ndi Timoteo, kwa Mpingo wa Atesalonika mwa Mulungu Atate wathu ndi Ambuye Yesu Kristu:
2 Cisomo kwa inu ndi mtendere wa kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Kristu.
3 Tiziyamika Mulungu nthawi zonse cifukwa ca inu, abale, monga kuyenera; pakuti cikhulupiriro canu cikula cikulire, ndipo cicurukira cikondanoca inu nonse, yense pa mnzace;
4 kotero kuti ife tokha tidzitamandira za inu m'Mipingo ya Mulungu, cifukwa ca cipiriro canu, ndi cikhulupiriro canu, m'mazunzo anu onse ndi zisautsozo muzimva;
5 ndico citsimikizo ca ciweruziro colungama ca Mulungu; kuti mu-kawerengedwe oyenera ufumu wa Mulungu, umenenso mumvera zowawa;
6 popeza nkolungama kwa Mulungu kubwezera cisautso kwa iwo akucitira inu cisautso,
7 ndi kwa inu akumva cisautso mpumulo pamodzi ndi ire, pa bvumbulutso la Ambuye Yesu wocokera Kumwamba pamodzi ndi angelo a mphamvu yace,
8 m'lawi lamoto, ndi kubwezera cilango kwa iwo osamdziwa Mulungu, ndi iwo osamvera Uthenga Wabwino wa Ambuye wathu Yesu;
9 amene adzamva cilango, ndico cionongeko cosatha cowasiyanitsa ku nkhope ya Ambuye, ndi ku ulemerero wa mphamvu yace,
10 pamene adzadza kudzalemekezedwa mwa oyera mtima ace, ndi kukhala wodabwizitsa mwa onse akukhulupirira (popeza munakhulupirira umboni wathu wa kwa inu) m'tsiku lija.
11 Kukatero tikupemphereraninso nthawi zonse, kuti Mulungu wathu akakuyeseni inu oyenera kuitanidwa kwanu, nakakwaniritse comkomera conse, ndi nchito ya cikhulupiriro mumphamvu;
12 kuti dzina la Ambuye wathu Yesu lilemekezedwe mwa inu, ndi inu mwa iye, monga mwa cisomo ca Mulungu wathu ndi Ambuye Yesu Kristu.
1 Ndipo tikupemphani, abale, cifukwa ca kudza kwace kwa Ambuye wathu Yesu Kristu, ndi kusonkhana pamodzi kwathu kwa iye;
2 kuti musamagwedezeka mtima msanga ndi kutaya maganizo anu, kapena kuopsedwa, mwa mzimu kapena mwa mau; kapena mwa kalata, monga wolembedwa ndi ife, monga ngati tsiku la Ambuye lafika;
3 munthu asakunyengeni konseko; kuti silifika, koma ciyambe cifike cipatukoco, nabvumbulutsike munthu wosayeruzika, mwana wa cionongeko,
4 amene atsutsana nazo, nadzikuza pa zonse zochedwa Mulungu, kapena zopembedzeka; kotero kuti iye wakhalapansi ku Kacisi wa Mulungu, nadzionetsera yekha kuti ali Mulungu.
5 Simukumbukila kodi, kuti pokhala nanu, ndisanacoke ine, ndinakuuzani izi?
6 Ndipo tsopano comletsa mucidziwa, kuti akabvumbulutsidwe iye m'nyengo yace ya iye yekha.
7 Pakuti cinsinsi ca kusayeruzika cayambadi kucita; cokhaci pali womletsa tsopano, kufikira akamcotsa pakati.
8 Ndipo pamenepo adzabvumbulutsidwa wosayeruzikayo, amene Ambuye Yesu adzamthera ndi mzimu wa pakamwa pace, nadzamuononga ndi maonekedwe a kudza kwace;
9 ndiye amene kudza kwace kuli monga mwa macitidwe a Satana, mu mphamvu yonse, ndi zizindikilo ndi zozizwa zonama;
10 ndi m'cinyengo conse ca cosalungama kwa iwo akuonongeka, popeza cikondi ca coonadi sanacisandira, kuti akapulumutsidwe iwo.
11 Ndipo cifukwa cace Mulungu atumiza kwa iwo macitidwe a kusoceretsa, kuti akhulupirire bodza;
12 kuti aweruzidwe onse amene sanakhulupirira coonadi, komatu anakondwera ndi cosalungama.
13 Koma tiyenera ife tiziyamika Mulungu nthawi zonse cifukwa: ca inu, abale okondedwa ndi Ambuye, kuti Mulungu anakusankhani inu kuyambira paciyambi, mulandire cipulumutso mwa ciyeretso ca Mzimu ndi cikhulupiriro ca coonadi;
14 kumene aoaitanako inu mwa Uthenga Wabwino wathu, kuti mulandire ulemerero wa Ambuye wathu Yesu Kristu.
15 Cifukwa cace tsono, abale, cirimikani, gwiritsani miyambo imene tinakuphunzitsani, kapena mwa mau, kapena mwa kalata wathu.
16 Ndipo Ambuye wathu Yesu Kristu, ndi Mulungu Atate wathu amene anatikonda natipatsa elsangalatso cosatha ndi ciyembekezo cokoma mwa cisomo,
17 asangalatse mitima yanu, nakhazikitse inu mu nchito yonse ndi mau onse abwino.
1 Cotsalira, abale, mutipempherere, kuti mau a Ambuye athamange, nalemekezedwe, monganso kwanu;
2 ndi kuti tilanditsidwe m'manja a anthu osayenerandi oipa; pakuti si onse ali naco cikhulupiriro.
3 Koma Ambuye ali wokhulupirika amene adzakukhazikitsani inu, nadzakudikirirani kuletsa woipayo;
4 koma tikhulupirira mwa Ambuye za inu, kuti mumacita, ndiponso mudzacita zimene tikulamulirani.
5 Ndipo Ambuye atsogolere bwino mitima yanu ilowe m'cikondi ca mulungu ndi m'cipiriro ca Kristu,
6 Ndipo tikulamulirani, abale, m'dzina la Ambuye wathu Yesu Kristu, kuti mubwebvuke kwa mbale yense wakuyenda dwacedwace, wosatsata mwambo umene anaulandira kwa ife.
7 Pakuti mudziwa nokha m'mene muyenera kutitsanza ifemo; pakuti sitinakhala dwacedwace mwa inu;
8 kapena sitinadya mkate cabe pa dzanja la munthu ali yense, komatu m'cibvuto ndi cipsinjo, tinagwira nchito usiku ndi usana, kuti tingalemetse wina wa inu;
9 si cifukwa tiribe ulamuliro, komatu kuti tidzipereke tokha tikhale kwa inu citsanzo canu, kuti mukatitsanze ife.
10 Pakutinso pamene tinali nanu tidakulamulirani ici, Ngati munthu safuna kugwira nchito, asadyenso.
11 Pakuti tikumva za ena mwa inu kuti ayenda dwacedwace, osagwira nchito konse, kama ali ocita mwina ndi mwina.
12 Koma oterewa tiwalamulira ndi kuwadandaulira mwa Ambuye Y esu Kristu, kuti agwire nchito pokhala cete, nadye cakudya cadwo okha,
13 Kama inu, abale, musaleme pakucita zabwino.
14 Koma ngati wina samvera mau athu m'kalata uyu, yang'anirani ameneyo, kuti musayanjane naye, kuti acite manyazi.
15 Koma musamuyese mdani, kama mumuyambirire ngati mbale.
16 Ndipo Ambuye wa mtendere yekha atipatse ife mtendere nthawi zonse, monsemo. Ambuye akhale ndi inu nonse.
17 Cilankhulo ndi dzanja langa Paulo; ndico cizindikilo m'kalata ali yense; ndiko kulemba kwanga.
18 Cisomo ca Ambuye wathu Yesu Kristu cikhale ndi inu nonse.