1

1 NDIPO Yehova ananena ndi Mose m'cipululu ca Sinai, m'cihema cokomanako, tsiku loyamba la mwezi waciwiri, caka caciwiri ataturuka m'dziko la Aigupto, ndi kuti,

2 Werenga khamu lonse la ana a Israyeli, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba ya makolo ao ndi kuwerenga maina ao, amuna onse mmodzi mmodzi.

3 Iwe ndi Aroni muwawerenge monga mwa magulu ao, onse m'Israyeli akuturuka kunkhondo, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu,

4 Ndipo pamodzi ndi inu pakhale munthu mmodzi wa mapfuko onse; yense mkuru wa nyumba ya kholo lace.

5 Ndipo maina a amuna amene aime nanu ndi awa: wa Rubeni, Elizuri mwana wa Sedeuri.

6 Wa Simeoni, Selumiyeli mwana wa Zurisadai.

7 Wa Yuda, Nahesoni mwana wa Aminadabu.

8 Wa Isakara, Netaneli mwana wa Zuwara.

9 Wa Zebuloni, Eliyabu mwana wa Heloni.

10 Wa ana a Yosefe: wa Efraimu, Elisama mwana wa Amihudi; wa Manase, Gamaliyeli mwana wa Pedazuri.

11 Wa Benjamini, Abidana mwana wa Gideoni.

12 Wa Dani, Ahiyezeri mwana wa Amisadai.

13 Wa Aseri, Pagiyeli mwana wa Okirani.

14 Wa Gadi, Eliyasafe mwana wa Deyueli.

15 Wa Nafitali, Ahira mwana wa Enani.

16 Iwo ndiwo oitanidwa a khamu, akalonga a mapfuko a makolo ao; ndiwo akuru a zikwizo za Israyeli.

17 Ndipo Mose ndi Aroni anatenga anthu awa, onenedwa maina ao;

18 nasonkhanitsa khamu lonse tsiku loyamba la mwezi waciwiri, ndipo iwo anawakumbira magwero ao kuchula mabanja ao, ndi nyumba za makolo ao, ndi kuwerenga maina kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu mmodzi mmodzi.

19 Monga Yehova anauza Mose, momwemo anawawerenga m'cipululu ca Sinai.

20 Ndipo ana a Rubeni, mwana woyamba wa Israyeli, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina mmodzi mmodzi, amuna onse kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

21 owerengedwa ao a pfuko la Rubeni, ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu ndi cimodzi kudza mazana asanu.

22 A ana a Simeoni, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, owerengedwa ao, powerenga maina mmodzi mmodzi, amuna onse kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

23 owerengedwa ao a pfuko la Simeoni, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi zinai kudza mazana atatu.

24 A ana a Gadi, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

25 owerengedwa ao a pfuko la Gadi, ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu kudza mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu.

26 A ana a Yuda, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makomi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

27 owerengedwa ao a pfuko la Yuda, ndiwo zikwi makumi asanu ndi awiri mphambu zinai kudza mazana asanu ndi limodzi.

28 A ana a Isakara, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

29 owerengedwa ao a pfuko la lsakara, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zinai kudza mazana anai.

30 A ana a Zebuloni, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

31 owerengedwa ao a pfuko la Zebuloni, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi ziwiri kudza mazana anai.

32 A ana a Yosefe, ndiwo a ana a Efraimu, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

33 owerengedwa ao a pfuko la Efraimu, ndiwo zikwi makumi anai mphambu mazana asanu.

34 A ana a Manase, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

35 owerengedwa ao a pfuko la Manase, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu ziwiri kudza mazana awiri.

36 A ana a Benjamini, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

37 owerengedwa ao a pfuko la Benjamini, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu zisanu kudza mazana anai.

38 A ana a Dani, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

39 owerengedwa ao a pfuko la Dani, ndiwo zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu ziwiri kudza mazana asanu ndi awiri.

40 A ana a Aseri, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

41 owerengedwa ao a pfuko la Aseri, ndiwo zikwi makumi anai mphambu cimodzi kudza mazana asanu.

42 A ana a Nafitali, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;

43 owerengedwa ao a pfuko la Nafitali, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zitatu kudza mazana anai.

44 Iwo ndiwo amene anawerengedwa, amene Mose anawerenga pamodzi ndi Aroni, ndi akalonga a Israyeli, ndiwo amuna khumi ndi awiri; yense kunenera nyumba ya kholo lace.

45 Potero owerengedwa onse a ana a Israyeli monga mwa nyumba za makolo ao, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo m'Israyeli;

46 inde owerengedwa onse ndiwo zikwi mazana asanu ndi limodzi mphambu zitatu kudza mazana asanu ndi makumi asanu.

47 Koma Alevi monga mwa pfuko la makolo ao sanawerengedwa mwa iwo.

48 Popeza Yehova adalankhula ndi Mose, ndi kuti,

49 Pfuko la Levi lokha usaliwerenge, kapena kuona kufikira kwao mwa ana a Israyeli;

50 koma iwe, uike Alevi asunge kacisi wa mboni, ndi zipangizo zace zonse, ndi zonse ali nazo; azinyamula kacisi, ndi zipangizo zace zonse; namtumikire, namange mahema ao pozungulira pa kacisi.

51 Ndipo akati amuke naye kacisiyo, Aleviamgwetse, ndipo akati ammange, Alevi amuimike; ndipo mlendo akayandikizako amuphe,

52 Ndipo ana a Israyeli amange mahema ao, yense ku cigono cace, ndi yense ku mbendera yace, monga mwa makamu ao.

53 Koma Alevi amange mahema ao pozungulira pa kacisi wa mboni, kuti mkwiyo ungagwere khamu la ana a Israyeli; ndipo Alevi azidikira kacisi wa mboni.

54 Momwemo ana a Israyeli anacita monga mwa zonse Yehova adauza Mosel anacita momwemo.

2

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,

2 Ana a Israyeli azimanga mahema ao yense ku mbendera yace, ya cizindikilo ca nyumba ya kholo lace; amange mahema ao popenyana ndi cihema cokomanako pozungulira.

3 Ndipo iwo akumanga mahema ao ku m'mawa koturuka dzuwa ndiwo a mbendera ya cigono ca Yuda, monga mwa makamu ao; ndipo kalonga wa ana a Yuda ndiye Nahesoni mwana wa Aminadabu.

4 Ndipo khamu lace, ndi owerengedwa ao, ndiwo zikwi makumi asanu ndi awiri, mphambu zinai, kudza mazana asanu ndi limodzi.

5 Ndipo iwo akumanga mahema ao poyandikizana naye ndiwo a pfuko la Isakara; ndipo kalonga wa ana a Isakara ndiye Netandi mwana wa Zuwara.

6 Ndipo khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zinai kudza mazana anai.

7 Ndi pfuko la Zebuloni: kalonga wa ana a Zebuloni ndiye Eliyabu mwana wa Heloni.

8 Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi ziwiri kudza mazana anai.

9 Owerengedwa onse a cigono ca Yuda ndiwo zikwi makumi khumi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza zisanu ndi cimodzi mphambu mazana anai, monga mwa makamu ao, Ndiwo azitsogolera ulendo.

10 Mbendera ya cigono ca Rubeni ikhale kumwera monga mwa makamu ao; ndipo kalonga wa ana a Rubeni ndiye Elizuri mwana wa Sedeuri.

11 Ndi khamu lace, ndi olembedwa ace, ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu ndi cimodzi kudza mazana asanu.

12 Ndipo iwo akumanga mahema ao poyandikizana naye ndiwo a pfuko la Simeoni; ndi kalonga wa ana a Simeoni ndiye Selumiyeli mwana wa Surisadai.

13 Ndi khamu lace ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zisanu ndi zinai kudza mazana atatu.

14 Ndi pfuko la Gadi; kalonga wa ana a Gadi ndiye Eliyasafe mwana wa Reueli.

15 Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu kudza mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu.

16 Owerengedwa onse a cigono ca Rubeni ndiwo zikwi makumi khumi mphambu makumi asanu ndi cimodzi kudza mazana anai mphambu makumi asanu, monga mwa makamu ao. Ndiwo azitsatana nao otsogolerawo.

17 Pamenepo khamu la Alevi azimuka naco cihema cokomanako, pakati pa makamu; monga amamanga mahema ao, momwemo azimuka ulendo wao, munthu yense pamalo pace, monga mwa mbendera zao.

18 Mbendera ya cigono ca Efraimu izikhala kumadzulo monga mwa makamu ao; ndipo kalonga wa ana a Efraimu ndiye Elisama mwana wa Amihudi.

19 Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi anai kudza mazana asanu.

20 Ndipo oyandikizana naye ndiwo a pfuko la Manase; ndi kalonga wa ana a Manase ndiye Gamaliyeli mwana wa Pedazuri.

21 Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu ziwiri kudza mazana awiri.

22 Ndi pfuko la Benjamini: kalonga wa ana a Benjamini ndiye Abidana mwana wa Gideoni.

23 Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu zisanu kudza mazana anai.

24 Owerengedwa onse a cigono ca Efraimu ndiwo zikwi makumi khumi mphambu zisanu ndi zitatu kudza zana limodzi, monga mwa makamu ao. Iwo ndiwo aziyenda gulu lacitatu paulendo.

25 Mbendera ya cigono ca Dani izikhala kumpoto monga mwa makamu ao; ndi kalonga wa ana a Dani ndiye Ahiyezeri mwana wa Amisadai.

26 Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu ziwiri kudza mazana asanu ndi awiri.

27 Ndipo iwo akumanga mahema ao poyandikizana naye ndiwo a pfuko la Aseri; ndi kalonga wa ana a Aseri ndiye Pagiyeli mwana wa Okirani.

28 Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi anai mphambu cimodzi kudza mazana asanu.

29 Ndi pfuko la Nafitali: ndi kalonga wa ana a Nafitali ndiye Ahira mwana wa Enani.

30 Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi asanu mphambu zitatu kudza mazana anai.

31 Owerengedwa onse a cigono ca Dani ndiwo zikwi makumi khumi mphambu makumi asanu kudza zisanu ndi ziwiri mphambu mazana asanu ndi Hmodzi. Iwo ndiwo aziyenda m'mbuyo paulendo, monga mwa mbendera zao.

32 Amenewo ndiwo anawerengedwa a ana a Israyeli monga mwa nyumba za makolo ao; owerengedwa onse a m'zigono, monga mwa makamu ao, ndiwo zikwi makumi khumi kasanu ndi kamodzi mphambu zitatu kudza mazana asanu ndi makumi asanu.

33 Koma sanawerenga Alevi mwa ana a Israyeli; monga Yehova adauza Mose.

34 Ndipo ana a Israyeli anacita monga mwa zonse Yehova adauza Mose, momwemo anamanga mahema ao pa mbendera zao, momwemonso anayenda paulendo, yense monga mwa mabanja ace, monga mwa nyumba za makolo ace.

3

1 Mibadwo ya Aroni ndi Mose, tsiku lija Yehova ananena ndi Mose m'phiri la Sinai, ndi iyo.

2 Ndipo maina ao a ana amuna a Aroni ndi awa: Woyamba Nadabu, ndi Abihu, Eleazara, ndi Itamara.

3 Awa ndi maina a ana amuna a Aroni, ansembe odzozedwawo, amene anawadzaza manja ao acite nchito ya nsembe.

4 Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamaso pa Yehova muja anabwera nao moto wacilendo pamaso pa Yehova, m'cipululu ca Sinai, ndipo analibe ana; koma Eleazara ndi Itamara anacita Debito ya nsembe pamaso pa atate wao Aroni.

5 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

6 Sendera nalo kuno pfuko la Levi, ndi kuwaika pamaso pa Aroni wansembe, kuti amtumikire.

7 Ndipo azisunga udikiro wace, ndi udikiro wa khamu lonse pa khomo la cihema cokomanako, kucita nchito ya kacisi.

8 Ndipo asunge zipangizo zonse za cihema cokomanako, ndi udikiro wa ana a Israyeli, kuicita nchito ya kacisi.

9 Ndipo uzipereka Alevi kwa Aroni ndi kwa ana ace amuna; apatsidwa kwa iye ndithu, ocokera kwa ana a Israyeli.

10 Koma uike Aroni ndi ana ace amuna, azisunga nchito yao ya nsembe; ndi mlendo wakusendera pafupi amuphe.

11 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

12 Ndipo taonani, Ine ndatenga Alevi kuwacotsa pakati pa ana a Israyeli m'malo mwa ana ovamba onse, oyamba kubadwa mwa ana a Israyeli; ndipo Aleviwo ndi anga.

13 Pakuti ana oyamba onse ndi anga; tsiku lija ndinakantha ana oyamba onse m'dziko la Aigupto ndinadzipatulira ana oyamba onse m'Israyeli, kuyambira munthu kufikira coweta; ndiwo anga; Ine ndine Yehova.

14 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'cipululu ca Sinai, nati,

15 Werenga ana a Levi monga mwa nyumba ya makolo ao, monga mwa mabanja ao; uwawerenge mwamuna yense wa mwezi umodzi ndi mphambu.

16 Ndipo Mose anawawerenga monga mwa mau a Yehova, monga adamuuza.

17 Ndipo ana a Levi maina ao ndi awa: Gerisoni, ndi Kohati ndi Merari.

18 Ndi ana a Gerisoni maina ao ndi awa, monga mwa mabanja ao: Libini, ndi Simei.

19 Ndi ana a Kohati monga mwa mabanja ao: Amiramu ndi lzara, Hebroni ndi Uziyeli.

20 Ndi ana a Merari monga mwa mabanja ao: Mali ndi Musi. Awa ndi mabanja a Alevi monga mwa nyumba za makolo ao.

21 Banja la Libini, ndi mabanja a Simei, ndiwo a Gerisoni; ndiwo mabanja a Gerisoni.

22 Owerengedwa ao, powawerenga amuna onse, kuyambira mwana wa mwezi umodzi ndi mphambu, owerengedwa ao ndiwo zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu mazana asanu.

23 Mabanja a Agerisoni azimanga mahema ao pambuyo pa kacisi kumadzulo.

24 Ndipo kalonga wa nyumba ya makolo a Agerisoni ndiye Eliyasafe mwana wa Layeli.

25 Ndipo udikiro wa ana a Gerisoni m'cihema cokomanako ndiwo kacisi, ndi cihema, cophimba cace, ndi nsaru yotsekera pa khomo la cihema cokomanako,

26 ndi nsaru zocinga za kubwalo, ndi nsaru yotsekera pa cipata ca pabwalo, lokhala kukacisi, ndi ku guwa la nsembe pozungulira, ndi zingwe zace za ku nchito zace zonse.

27 Banja la Aamiramu, ndi banja la Aizara, ndi banja la Ahebroni, ndi banja la Auziyeli ndiwo a Kohati; ndiwo mabanja a Akohati.

28 Powawerenga amuna onse, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu ndiwo zikwi zisanu ndi zitatu mphambu mazana asanu ndi limodzi, akusunga udikiro wa pa malo opatulika.

29 Mabanja a ana a Kohati azimanga mahema ao pa mbali ya kacisi ya kumwera.

30 Ndipo kalonga wa nyumba ya makolo ao ya mabanja a Akohati ndiye Elizafana mwana wa Uziyeli.

31 Ndipoudikirowaondiwo likasa, ndi gome, ndi coikapo nyali, ndimagome a nsembe, ndi zipangizo za malo opatulika zimene acita nazo, ndi nsaru yocinga, ndi nchito zace zonse.

32 Ndipo kalonga wa akalonga a Alevi ndiye Eleazara mwana wa Aroni wansembeyo; ndiye aziyang'anira osunga udikiro wa pa malo opatulika.

33 Banja la Amali, ndi banja la Amusi ndiwo a Merari; ndiwo mabanja a Merari.

34 Ndipo owerengedwa ao, powerenga amuna onse, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu, ndiwo zikwi zisanu ndi cimodzi kudza mazana awiri.

35 Ndi kalonga wa nyumba ya makolo ya mabanja a Merari ndiye Zuriyeli mwana wa Abiyaili; azimanga mahema ao pa mbali ya kacisi ya kumpoto.

36 Ndipo coyang'anira iwo, udikiro wao wa ana a Merari ndiwo matabwa a kacisi, ndi mitanda yace, ndi mizati ndi nsanamira zace, ndi makamwa ace, ndi zipangizo zace zonse, ndi nchito zace zonse;

37 ndi nsici za pabwalo pozungulira, ndi makamwa ace, ndi ziciri zace, ndi zingwe zace.

38 Ndipo amene adamanga mahema ao pa khomo la kacisi, kum'mawa, pa khomo la cihema cokomanako koturukira dzuwa, ndiwo Mose ndi Aroni, ndi ana ace amuna, akusunga udikiro wa malo opatulika, ndiwo udikiro wa ana a Israyeli; koma mlendo wakuyandikizako amuphe,

39 Owerengedwa onse a Alevi, adawawerenga Mose ndi Aroni, powauza Yehova, monga mwa mabanja ao, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu, ndiwo zikwi makumi awiri mphambu ziwiri.

40 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Werenga amuna oyamba kubadwa onse a ana a Israyeli kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu nuone ciwerengo ca maina ao.

41 Ndipo unditengere Ine Alevi (ine ndine Yehova) m'malo mwa oyamba kubadwa onse mwa ana a Israyeli; ndi ng'ombe za Alevi m'malo mwa zoyamba kubadwa zonse mwa ng'ombe za ana a Israyeli.

42 Ndipo Mose anawawerenga, monga Yehova adamuuza, oyamba kubadwa onse mwa ana a Israyeli.

43 Ndipo amuna onse oyamba kubadwa, powerenga maina, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu, owerengedwa ao, ndiwo zikwi makumi awiri mphambu ziwiri kudza mazana awiri ndi makumi asanu ndi awiri mphambu atatu.

44 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

45 Landira Alevi m'malo mwa oyamba kubadwa onse mwa ana a Israyeli, ndi ng'ombe za Alevi m'malo mwa ng'ombe zao; ndipo Alevi azikhala anga; Ine ndine Yehova.

46 Kunena za mazana awiri ndi makumi asanu ndi awiri kudza atatuwo oyamba kubadwa a ana a Israyeli, akuposa Alevi, akaomboledwe,

47 ulandire masekeli asanu pa munthu mmodzi; uwalandire pa muyeso wa sekeli wa malo opatulika (sekeli ndiwo magera makumi awiri);

48 nupereke ndarama zimene akuposawo anaomboledwa nazo kwa Aroni ndi kwa ana ace amuna.

49 Pamenepo Mose analandira ndarama zaom bola nazo kwa iwo akuposa aja adawaombola Alevi;

50 analandira ndaramazo kwa oyamba kubadwa a ana a Israyeli; masekeli cikwi cimodzi mphambu mazana atatu kudza makumi asanu ndi limodzi mphambu asanu, kuyesa sekeli wa malo opatulika.

51 Ndipo Mose anapatsa Aroni ndi ana ace ndarama zaom bola nazo monga mwa mau a Yehova, monga Yehova adauza Mose.

4

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,

2 Werengani ana a Kohati pakati pa ana a Levi, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao,

3 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu, kufikira zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu, kuti agwire nchito ya cihema cokomanako.

4 Nchito ya ana a Kohati m'cihema cokomanako ndi iyi, kunena za zinthu zopatulikitsa:

5 akati amuke a m'cigono, Aroni ndi ana ace amuna azilowa, natsitse nsaru yocinga, ndi kuphimba nayo likasa la mboni,

6 ndi kuikapo cophimba ca zikopa za akatumbu; ndi kuyalapo nsaru yamadzi yeni yeni, ndi kupisako mphiko zace.

7 Ndi pa gome la mkate waonekera ayale nsaru yamadzi, naikepo mbale zace, ndi zipande, ndi mitsuko, ndi zikho zakuthira nazo; mkate wa cikhalire uzikhalaponso.

8 Ndipo ayale pa izi nsaru yofiira, ndi kuliphimba ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kupisako mphiko zace.

9 Ndipo atenge nsaru yamadzi, ndi kuphimba coikapo nyali younikira, ndi nyali zace, ndi mbano zace, ndi zaolera zace, ndi zotengera zace zonse za mafuta zogwira nazo nchito yace.

10 Ndipo acimange ndi cipangizo zace zonse m'cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kuziika pa conyamulira.

11 Ndipo pa guwa la nsembe lagolidi aziyala nsaru yamadzi, naliphimbe ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kupisako mphiko zace.

12 Natenge zipangizo zace zonse za utumiki, zimene atumikira nazo m'malo opatulika, nazimange m'nsaru yamadzi, ndi kuziphimba ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kuziika paconyamulira.

13 Ndipo azicotsa mapulusa pa guwa la nsembe, ndi kuyala pa ilo nsaru yofiirira.

14 Naikepo zipangizo zace zonse, zimene atumikira nazo pamenepo, mbale za zofukiza, mitungo, ndi zaolera, ndi mbale zowazira, zipangizo zonse za guwa la nsembe; nayalepo cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kupisako mphiko zace.

15 Atatha Aroni ndi ana ace amuna kuphimba malo opatulika, ndi zipangizo zace zonse za malo opatulika, pofuna kumuka am'cigono; atatero, ana a Kohati adze kuzinyamula; koma asakhudze zopatulikazo, kuti angafe. Zinthu izi ndizo akatundu a ana a Kohati m'cihema cokomanako.

16 Ndipo zoyang'anira Eleazara, mwana wa Aroni wansembe, ndizo mafuta a nyaliyo, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsembe yaufa kosalekeza, ndi mafuta odzoza, udikiro wa kacisi wonse, ndi zonse ziri m'mwemo, malo opatulika, ndi zipangizo zace.

17 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, Dati,

18 Musamasadza pfuko la mabanja a Kohati kuwacotsa pakati pa Alevi;

19 koma muzitero nao kuti akhale ndi moyo, osafa ai, poyandikiza iwo zopatulikitsazo; Aroni ndi ana ace amuna alowe, namuikire munthu yense nchito yace ndi katundu wace.

20 Koma asalowe kukaona zopatulikazo pozikulunga, kuti angafe.

21 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

22 Werenganso ana a Gerisoni, monga mwa nyumba za makolo ao, monga mwa mabanja ao.

23 Uwawerenge kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu, kufikira a zaka makumi asanu; onse akulowa kutumikira utumikiwo, kucita nchitoyi m'cihema cokomanako.

24 Nchito ya mabanja a Agerisoni, pogwira nchito ndi kusenza katundu ndi iyi;

25 azinyamula nsaru zophimba za kacisi, ndi cihema cokomanako, cophimba cace, ndi cophimba ca zikopa za akatumbu ciri pamwamba pace, ndi nsaru yotsekera pa khomo la cihema cokomanako;

26 ndi nsaru zocingira za pabwalo, ndi nsaru yotsekera ku cipata ca pabwalo liri pakacisi ndi pa guwa la nsembe pozungulira, ndi zingwe zao, ndi zipangizo zonse za Debito zao, ndi zonse acita nazo; m'menemo muli nchito zao.

27 Nchito yonse ya ana a Agerisoni, kunena za akatundu ao ndi nchito zao zonse, ikhale monga adzanena Aroni ndi ana ace amuna; ndipo muwaike adikire akatundu ao onse.

28 Iyi ndi nchito ya mabanja a ana a Gerisoni m'cihema cokomanako; ndipo Itamara mwana wa Aroni wansembe ayang'anire udikiro wao.

29 Kunena za ana a Merari, Uwawerenge monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao.

30 Uwawerenge kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu, kucita nchito ya cihema cokomanako.

31 Ndipo udikiro wa akatundu ao, monga mwa nchito zao zonse m'cihema cokomanako ndi ici: matabwa a kacisi, ndi mitanda yace, ndi mizati ndi nsanamira zace, ndi makamwa ace;

32 ndi nsici za kubwalo kozungulira, ndi makamwa ace, ndi ziciri zace, ndi zingwe zace, pamodzi ndi zipangizo zace zonse, ndi nchito yace yonse; ndipo muziwerenga zipangizo za udikiro wa akatundu ao ndi kuwaehula maina ao.

33 Iyi ndi nchito ya mabanja a ana a Merari, monga mwa nchito zao zonse m'cihema cokomanako, mowauza Itamara mwana wa Aroni wansembe.

34 Ndipo Mose ndi Aroni ndi akalonga a khamu anawerenga ana a Akohati monga mwa mabanja ao, ndi monga mwa nyumba za makolo ao,

35 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu, kuti agwire Debito m'cihema cokomanako;

36 ndipo owerengedwa ao monga mwa mabanja ao ndiwo zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu.

37 Awa ndi owerengedwa a mabanja a Akohati, onse akutumikira m'cihema cokomanako, amene Mose ndi Aroni anawawerenga monga mwa mau a Yehova mwa dzanja la Mose.

38 Ndipo ana owerengedwa a Gerisoni, monga mwa mabanja ao, ndi monga mwa nyu mba za makolo ao,

39 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu, kuti agwire nchito m'cihema cokomanako,

40 owerengedwa ao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, ndiwo zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi limodzi kudza makumi atatu.

41 Amenewo ndiwo owerengedwa a mabanja a ana a Gerisoni, onse akutumikira m'cihema cokomanako, adawawerenga Mose ndi Aroni monga mwa mau a Yehova.

42 Ndipo owerengedwa a mabanja a ana a Merari, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao,

43 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa utumikiwu kuti agwire nchito m'cihema cokomanako,

44 owerengedwa ao monga mwa mabanja ao, ndiwo zikwi zitatu ndi mazana awiri.

45 Amenewo ndiwo owerengedwa a mabanja a ana a Merari, amene Mose ndi Aroni anawawerenga monga mwa mau a Yehova mwa dzanja la Mose.

46 Owerengedwa onse a Alevi, amene Mose ndi Aroni ndi akalonga a Israyeli anawawerengera, monga mwa mabanja ao, ndi monga mwa nyumba za makolo ao,

47 kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu kufikira a zaka makumi asanu, onse akulowa kugwira nchito ya utumikiwu, ndiyo nchito ya akatundu m'cihema cokomanako;

48 owerengedwa ao ndiwo zikwi zisanu ndi zitatu kudza mazana asanu mphambu makumi asanu ndi atatu.

49 Anawawerenga monga mwa mau a Yehova ndi dzanja la Mose, onse monga mwa nchito zao, ndi monga mwa akatundu ao; anawawerenga monga momwe Yehova adauza Mose.

5

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

2 Uza ana a Israyeli kuti aziturutsa m'cigono akhate onse, ndi onse akukhala nako kukha, ndi onse odetsedwa cifukwa ca akufa;

3 muwaturutse amuna ndi akazi muwaturutsire kunja kwa cigono, kuti angadetse cigono cao, cimene ndikhala m'kati mwacemo.

4 Ndipo ana a Israyeli anacita cotero, nawaturutsira kunja kwa cigono; monga Yehova adanena ndi Mose momwemo ana a Israyeli anacita.

5 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

6 Nena ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Mwamuna kapena mkazi akacita cimo liri lonse amacita anthu, kucita mosakhulupirika pa Yehova, nakaparamuladi;

7 azibvomereza cimo lace adalicita; nabwezere coparamulaco monsemo, naonjezeko limodzi la magawo asanu, ndi kucipereka kwa iye adamparamulayo.

8 Koma munthuyo akapanda kukhala nayo nkhoswe imene akaibwezere coparamulaco, coparamula acibwezera Yehovaco cikhale ca wansembe; pamodzi ndi nkhosa yamphongo ya cotetezerapo, imene amcitire nayo comtetezera.

9 Ndipo nsembe zokweza zonse za zinthu zopatulika za ana a Israyeli, zimene abwera nazo kwa wansembe zisanduka zace.

10 Zopatulika za munthu ali yense ndi zace: ziti zonse munthu ali yense akapatsa wansembe, zasanduka zace.

11 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

12 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mkazi wa mwini akapatukira mwamuna wace, nakamcitira mosakhulupirika,

13 ndi munthu akagona naye, koma kumbisikira maso a mwamuna wace, ndikumng'unira; nadetsedwa mkaziyo, koma palibe mboni yomtsutsa, kapena sanamgwira alimkucita;

14 ndipo ukamgwira mwamuna mtima wansanje, kuti acitire nsanje mkazi wace, popeza wadetsedwa; kapena ukamgwira mtima wansanje, kuti amcitire mkazi wace nsanje angakhale sanadetsedwa;

15 pamenepo mwamunayo azidza naye mkazi wace kwa wansembe, nadze naco copereka cace, limodzi la magawo khumi la efa wa ufa wabarele; asathirepo mafuta, kapena kuikapo libano; popeza ndiyo nsembe yaufa yansanje, nsembe yaufa yacikumbutso, yakukumbutsa mphulupulu.

16 Ndipo wansembe abwere naye, namuike pamaso pa Yehova;

17 natenge madzi opatulika m'mbale yadothi wansembeyo, natengeko pfumbi liri pansi m'kacisi, wansembeyo nalithire m'madzimo.

18 Pamenepo wansembeyo aike mkaziyo pamaso pa Mulungu, nabvula mutu wa mkaziyo, naike nsembe yaufa yacikumbutso m'manja mwace, ndiyo nsembe yaufa yansanje; ndipo m'manja mwace mwa wansembe muzikhala madzi owawa akudzetsa temberero.

19 Ndipo wansembe amlumbiritse, nanene kwa mkazi, Ngati sanagona nawe munthu mmodzi yense, ngati sunapatukira kucidetso, pokhala ndiwe wa mwamuna wako, upulumuke ku madzi owawa awa akudzetsa temberero.

20 Koma iwe, ngati wapatukira mwamuna wako, ngati wadetsedwa, kuti wagona nawe munthu, wosati mwamuna wako;

21 pamenepo wansembe alumbiritse mkazi lumbiro lakutemberera, ndi wansembe anene kwa mkazi, Yehova akuike ukhale temberero ndi lumbiro pakati pa anthu a mtundu wako, pakuondetsa Yehova m'cuuno mwako, ndi kukutupitsa mbulu;

22 ndipo madzi awa akudzetsa temberero adzalowa m'matumbo mwako, nadzakutupitsa mbulu ndi kuondetsa m'cuuno mwako; ndipo mkaziyo aziti, Amen, Amen.

23 Ndipo wansembe alembere matemberero awa m'buku, ndi kuwafafaniza ndi madzi owawawa.

24 Ndipo amwetse mkaziyo madzi owawa akudzetsa temberero; ndi madzi odzetsa temberero adzalowa mwa iye nadzamwawira.

25 Ndipo wansembe atenge nsembe yaufa m'manja mwa mkazi, naweyule nsembe yaufa pamaso pa Yehova, nabwere nayo ku guwa la nsembe.

26 Wansembe atengekonso nsembe yaufa wodzala manja, cikumbutso cace, nacitenthe pa guwa la nsembe; ndipo atatero amwetse mkazi madziwo.

27 Ndipo atammwetsa madziwo, kudzatero, ngati wadetsedwa, nacita mosakhulupitika pa mwamuna wace, madzi odzetsa tembererowo adzalowa mwa iye nadzamwawira, nadzamtupitsa mbulu, ndi m'cuuno mwace mudzaonda; ndi mkaziyo adzakhala temberero pakati pa anthu a mtundu wace.

28 Koma ngati mkazi sanadetsedwa, nakhala woyera, pamenepo adzapulumuka, nadzaima.

29 Ici ndi cilamulo ca nsanje, pamene mkazi, pokhala naye mwamuna wace, ampatukira nadetsedwa;

30 kapena pamene mtima wansanje umgwira mwamuna, ndipo acitira mkazi wace nsanje; pamenepo aziika mkazi pamaso pa Yehova, ndipo wansembe amcitire cilamulo ici conse.

31 Mwamunayo ndiye wosacita mphulupulu, koma mkazi uyo asenze mphulupulu yace.

6

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mwamuna kapena mkazi akadzipatulira kulonieza cowinda ca Mnaziri, kudzipatulira kwa Yehova;

3 azisala vinyo ndi kacasu; asamwe vinyo wosasa, kapena kacasu wosasa, kapena cakumwa conse ca mphesa, asamwe; asadye mphesa zaziwisi kapena zouma.

4 Masiku onse a kusala kwace asadye kanthu kopangika ndi mphesa, kuyambira nthanga zace kufikira khungu lace,

5 Masiku onse a cowinda cace cakusala, lumo lisapite pamutu pace; kufikira adatha masikuwo adadzipatulira kwa Yehova, azikhala wopatulika; aleke nzera za tsitsi lace zimeretu.

6 Masiku onse akudzipatulira kwa Yehova asayandikize mtembo.

7 Asadzidetse ndi atate wace, kapena mai wace, mbale wace, kapena mlongo wace, akafa iwowa; popeza cowindira Mulungu wace ciri pamutu pace.

8 Masiku onse a kusala kwace akhala wopatulikira kwa Yehova.

9 Munthu akafa cikomo pali iye, ndipo akadetsa mutu wace wowinda; pamenepo azimeta mutu wace tsiku la kumyeretsa kwace, tsiku lacisanu ndi ciwiri aumete.

10 Ndipo tsiku lacisanu ndi citato adze nazo njiwa ziwiri, kapena maunda awiri, kwa wansembe, ku khomo la cihema cokomanako;

11 ndipo wansembe akonze imodzi nsembe yaucimo, ndi yina nsembe yopsereza, namtetezere popeza anacimwa nao mtembowo; ndipo apatulire mutu wace tsiku lomwelo.

12 Ndipo awapatulire Yehova masiku a kusala kwace, nadze nayo nkhosa yamphongo ya caka cimodzi ikhale nsembe yoparamula; koma masiku adapitawa azikhala cabe, popeza anadetsa kusala kwace.

13 Ndipo cilamulo ca Mnaziri, atatha masiku a kusala kwace ndi ici: azidza naye ku khomo la cihema cokomanako;

14 pamenepo abwere naco copereka cace kwa Yehova, nkhosa yamphongo ya caka cimodzi yopanda cirema, ikhale nsembe yopsereza, ndi nkhosa yamsoti yopanda cirema ikhale nsembe yaucimo, ndi nkhosa yamphongo yopanda cirema ikhale nsembe yoyamika;

15 ndi mtanga wa mkate wopanda cotupitsa, timitanda ta ufa wosalala tosanganiza ndi mafuta, ndi timitanda taphanthi todzoza ndi mafuta, ndi nsembe yao yaufa, ndi nsembe zao zothira.

16 Ndipo wansembe azibwera nazo pamaso pa Yehova, nakonze nsembe yace yaucimo, ndi nsembe yace yopsereza;

17 naphe nkhosa yamphongo yoyamika ya Yehova, pamodzi ndi mtanga wa mkate wopanda cotupitsa; wansembe akonzenso nsembe yace yaufa, ndi nsembe yace yothira.

18 Pamenepo Mnaziriyo amete mutu wace wa kusala kwace pa khomo la cihema cokomanako, natenge tsitsi la pa mutu wace wa kusala, naliike pamoto wokhala pansi pa nsembe yoyamika.

19 Ndipo wansembe atenge mwendo wamwamba wophika wa nkhosa yamphongo, ndi kamtanda kamodzi kopanda cotupitsa ka m'mtanga, ndi kamtanda kaphanthi kopanda cotupitsa kamodzi, ndi kuziika m'manja mwa Mnaziri, atameta kusala kwace;

20 ndipo wansembe aziweyula nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ici ncopatulikira wansembe, pamodzi ndi nganga ya nsembe yoweyula, pamodzi ndi mwendo wa nsembe yokweza; ndipo atatero Mnaziri amwe vinyo.

21 Ici ndi cilamulo ca Mnaziri wakuwinda, ndi ca copereka cace ca Yehova cifukwa ca kusala kwace, pamodzi naco cimene dzanja lace likacipeza; azicita monga mwa cowinda cace anaciwinda, mwa cilamulo ca kusala.

22 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

23 Nena ndi Aroni ndi ana ace, ndi kuti, Uzidalitsa ana a Israyeli motero; uziti nao,

24 Yehova akudalitse iwe, nakusunge;

25 Yehova awalitse nkhope yace pa iwe, nakucitire cisomo;

26 Yehova akweze nkhope yace pa iwe, nakupatse mtendere.

27 Potero aike dzina langa pa ana a Israyeli; ndipo ndidzawadalitsa.

7

1 Ndipo kunali kuti tsiku lomwe Mose anatsiriza kumuutsa kacisi, namdzoza ndi kumpatula, ndi zipangizo zace zonse, ndi guwa la nsembe, ndi zipangizo zace zonse, nazidzoza ndi kuzipatula;

2 akalonga a Israyeli, akuru a nyumba za makolo ao, anapereka nsembe, ndiwo akalonga a mapfuko akuyang'anira owerengedwa;

3 anadza naco copereka cao pamaso pa Yehova, magareta ophimbika asanu ndi mmodzi, ndi ng'ombe khumi ndi ziwfri; akalonga awiri anapereka gareta mmodzi, ndi kalonga mmodzi ng'ombe imodzi; nabwera nazo pakhomo pa kacisi.

4 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

5 Uzilandira kwa iwo, kuti zikhale zakucitira nchito ya cihema cokomanako; nuzipereke kwa Alevi, yense monga mwa nchito yace.

6 Ndipo Mose analandira magareta ndi ng'ombe, nazipereka kwa Alevi.

7 Anapatsa ana a Gerisoni magareta awiri ndi ng'ombe zinai, monga mwa nchito yao;

8 napatsa ana a Merari magareta anai ndi ng'ombe zisanu ndi zitatu, monga mwa nchito yao; wakuziyang'anira ndiye Itamara mwana wa Aroni wansembe.

9 Koma sanapatsa ana a Kohati kanthu; popeza nchito yao ndiyo ya zinthu zopatulika, zimene amazisenza pa mapewa ao.

10 Ndipo akalonga anabwera nazo za kupereka ciperekere guwa la nsembe tsiku lodzozedwa ili; inde akalongawo anabwera naco copereka cao pa guwa la nsembelo.

11 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Akalonga onse, yense pa tsiku lace, apereke zopereka zao za kupereka ciperekere guwa la nsembe.

12 Wakubwera naco copereka cace tsiku loyamba ndiye Nahesoni mwana wa Aminadabu, wa pfuko la Yuda:

13 copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace ndiko masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwirizo zodzala ndi ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta ukhale nsembeyaufa;

14 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

15 ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

16 ronde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

17 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa: asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Nahesoni mwana wa Aminadabu.

18 Tsiku laciwiri Netaneli mwana wa Zuwara, kalonga wa Isakara, anabwera naco cace:

19 anabwera naco copereka cace mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

20 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

21 ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

22 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

23 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Netaneli mwana wa Zuwara.

24 Tsiku lacitatu kalonga wa ana a Zebuloni, ndiye Eliyabu mwana wa Heloni:

25 copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

26 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

27 ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

28 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

29 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Eliyabu mwana wa Heloni.

30 Tsiku lacinai Elizuri, mwana wa Sedeuri, kalonga wa ana a Rubeni:

31 copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika, zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

32 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

33 ng'ombe yamphongo Imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

34 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

35 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Elizuri mwana wa Sedeuri.

36 Tsiku lacisanu kalonga wa ana a Simeoni, ndiye Selumiyeli, mwana wa Zurisadai:

37 copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

38 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

39 ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

40 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

41 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Selumiyeli mwana wa Zurisadai.

42 Tsiku lacisanu ndi cimodzi, kalonga wa ana a Gadi, Eliyasafe mwana wa Deyueli:

43 copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu; mbale yowazira Imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

44 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

45 ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

46 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

47 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Eliyasafe mwana wa Deyueli.

48 Tsiku lacisanu ndi ciwiri kalonga wa ana a Efraimu Elisama mwana wa Amihudi:

49 copereka cace mbizi Imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

50 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

51 ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

52 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

53 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa za mphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Elisama mwana wa Amihudi.

54 Tsiku lacisanu ndi citatu kalonga wa ana a Manase ndiye Gamaliyeli mwana wa Pedazuri:

55 copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

56 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

57 ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

58 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

59 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Gamaliyeli mwana wa Pedazuri.

60 Tsiku lacisanu ndi cinai kalonga wa ana a Benjamini, ndiye Abidana mwana wa Gideoni:

61 copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

62 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

63 ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

64 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

65 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Abidana mwana wa Gideoni.

66 Tsiku lakhumi kalonga wa ana a Dani, ndiye Ahiyezeri mwana wa Amisadai:

67 copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta ukhale nsembe yaufa;

68 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

69 ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

70 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

71 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Ahiyezeri mwana wa Amisadai.

72 Tsiku la khumi ndi limodzi kalonga wa ana a Aseri, ndiye Pagiyeli mwana wa Okirani;

73 copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

74 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

75 ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

76 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

77 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ndico copereka ca Pagiyeli mwana wa Okirani.

78 Tsiku lakhumi ndi ciwiri kalonga wa ana a Nafitali, ndiye Ahira mwana wa Enani:

79 copereka cace ndico mbizi imodzi yasiliva, kulemera kwace masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, mbale yowazira imodzi yasiliva ya masekeli makumi asanu ndi awiri, kuyesa sekeli wa malo opatulika; zonse ziwiri zodzala ndi ufa wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa;

80 cipande cimodzi cagolidi ca masekeli khumi, codzala ndi cofukiza;

81 ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, mwana wa nkhosa mmodzi wa caka cimodzi, zikhale nsembe yopsereza;

82 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo;

83 ndi nsembe yoyamika, ng'ombe ziwiri, nkhosa zamphongo zisanu, atonde asanu, ana a nkhosa asanu a caka cimodzi; ici ndi copereka ca Ahira mwana wa Enani.

84 Uku ndi kupereka ciperekere guwa la nsembe, ndi akalonga a Israyeli, tsiku la kudzoza kwace: mbizi zasiliva khumi ndi ziwiri, mbale zowazira zasiliva khumi ndi ziwiri, zipande zagolidi khumi ndi ziwiri;

85 mbizi yasiliva yonse masekeli zana limodzi ndi makumi atatu, ndi mbale yowazira yonse masekeli makumi asanu ndi awiri; siliva wonse wa zotengerazo ndizo masekeli zikwi ziwiri ndi mazana anai, kuyesa sekeli wa malo opatulika.

86 Zipande zagolidi ndizo khumi ndi ziwiri, zodzala ndi cofukiza, cipande conse masekeli khumi, kuyesa sekeli wa malo opatulika; golidi wonse wa zipandezo ndiwo masekeli zana limodzi ndi makumi awiri;

87 ng'ombe zonse za nsembe yopsereza ndizo ng'ombe khumi ndi ziwiri, nkhosa zamphongo khumi ndi ziwiri, ana a nkhosa a caka cimodzi khumi ndi awiri, pamodzi ndi nsembe yao yaufa; ndi atonde a nsembe zaucimo khumi ndi awiri;

88 ndi ng'ombe zonse za nsembe yoyamika ndizo ng'ombe makumi awiri ndi zinai, nkhosa zamphongo makumi asanu ndi limodzi, atonde makumi asanu ndi limodzi, ana a nkhosa a caka cimodzi makumi asanu ndi limodzi. Uku ndi kupereka ciperekere, litadzozedwa guwa la nsembe.

89 Ndipo polowa Mose ku cihema cokomanako, kunena ndi iye, anamva Mau akunena naye ocokera ku cotetezerapo ciri pa likasa la mboni, ocokera pakati pa akerubi awiriwo; ndipo iye ananena naye.

8

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Nena kwa Aroni, nuti naye, Pamene uyatsa nyalizo, nyali manu ndi ziwirizo ziwale pandunji pace pa coikapo nyalico.

3 Ndipo Aroni anacita cotero; anayatsa nyalizo kuti ziwale pandunji pace pa coikapo nyali, monga Yehova adauza Mose.

4 Ndipo mapangidwe ace a coikapo nyali ndiwo golidi wosula; kuyambira tsinde lace kufikira maluwa ace anacisula; monga mwa maonekedwe ace Yehova anaonetsa Mose, momwemo anacipanga coikapo nyali.

5 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

6 Uwatenge Alevi pakati pa ana a Israyeli, nuwayeretse.

7 Ndipo utere nao kuwayeretsa: uwawaze madzi akucotsa zoipa, ndipo apititse lumo pa thupi lao lonse, natsuke zobvala zao, nadziyeretse.

8 Pamenepo atenge ng'ombe yamphongo ndi nsembe yace yaufa, ufa wosanganiza ndi mafuta; utengenso ng'ombe yamphongo yina ikhale nsembe yaucimo.

9 Ndipo ubwere nao Alevi pakhomo pa cihema cokomanako; nuwasonkhanitse khamu lonse la ana a Israyeli;

10 nubwere nao Alevi pamaso pa Yehova; ndi ana a Israyeli aike manja ao pa Alevi;

11 ndi Aroni apereke Alevi ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova, yocokera kwa ana a Israyeli, kuti akhale akucita nchito ya Yehova,

12 Ndipo Alevi aike manja ao pa mitu ya ng'ombezo; pamenepo ukonze imodzi ikhale nsembe yaucimo, ndi inzace, nsembe yopsereza za Yehova, kucita cotetezera Alevi.

13 Ndipo uimike Alevi pamaso pa Aroni, ndi pamaso pa ana ace, ndi kuwapereka ngati nsembe yoweyula kwa Yehova.

14 Momwemo upatule Alevi mwa ana a Israyeli; kuti Alevi akhale anga.

15 Ndipo atatero alowe Alevi kucita Debito ya cihema cokomanako; ndipo uwayeretse, ndi kuwapereka ngati nsembe yoweyula.

16 Pakuti aperekedwa konse kwa Ine ocokera mwa ana a Israyeli; ndadzitengera iwo m'malo mwa onse akutsegula m'mimba, ndiwo oyamba kubadwa a ana a Israyeli.

17 Pakuti a oyamba kubadwa onse mwa ana a Israyeli ndi anga, mwa anthu ndi zoweta; tsiku lija ndinakantha oyamba kubadwa onse m'dziko la Aigupto, ndinadzipatulira iwo akhale anga.

18 Ndipo ndatenga Alevi m'malo mwa oyamba kubadwa onse mwa ana a Israyeli.

19 Ndipo ndapereka Alevi akhale mphatso ya kwa Aroni ndi ana ace amuna yocokera mwa ana a Israyeli, kucita nchito ya ana a Israyeli, m'cihema cokomanako ndi kucita cotetezera ana a Israyeli; kuti pasakhale mliri pakati pa ana a Israyeli, pakuyandikiza ana a Israyeli ku malo opatulika.

20 Ndipo Mose ndi Aroni ndi khamu lonse la ana a Israyeli anacitira Alevi monga mwa zonse Yehova adauza Mose kunena za Alevi; momwemo ana a lsrayeli anawacitira.

21 Ndipo Alevi anadziyeretsa, natsuka zobvala zao; ndi Aroni anawapereka ngati nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ndi Aroni anawacitira cotetezera kuwayeretsa.

22 Ndipo atatero, Alevi analowa kucita Debito yao m'cihema cokomanako pamaso pa Aroni, ndi pamaso pa ana ace amuna; monga Yehova anauza Mose kunena za Alevi, momwemo anawacitira.

23 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

24 Ici ndi ca Alevi: kuyambira ali wa zaka makumi awiri ndi zisanu ndi mphambu azilowa kutumikira utumikiwu mu nchito ya cihema cokomanako;

25 ndipo kuyambira zaka makumi asanu azileka kutumikira utumikiwu, osacitanso nchitoyi;

26 koma atumikire pamodzi ndi abale ao m'cihema cokomanako, kusunga udikirowo, koma osagwira nchito. Utere nao Alevi kunena za udikiro wao.

9

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'cipululu ca Sinai, mwezi woyamba wa caka caciwiri ataturuka m'dziko la Aigupto, ndi kuti,

2 Ana a Israyeli acite Paskha pa nyengo yoikidwa.

3 Tsiku lakhumi ndi cinai la mweziwo, madzulo, muziucita, pa nyengo yace yoikidwa; muucite monga mwa malemba ace onse, ndi maweruzo ace onse.

4 Ndipo Mose ananena ndi ana a Israyeli, kuti acite Paskha.

5 Ndipo anacita Paskha mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi cinai la mweziwo, madzulo, m'cipululu ca Sinai; monga mwa zonse Yehova adauza Mose, momwemo ana a Israyeli anacita.

6 Pamenepo panali amuna, anadetsedwa ndi mtembo wa munthu, ndipo sanakhoza kucita Paskha tsiku lomwelo; m'mwemo anafika pamaso pa Mose ndi pamaso pa Aroni tsiku lomwelo;

7 nanena naye amunawa, Tadetsedwa ife ndi mtembo wa munthu; atiletseranji, kuti tisabwere naco copereka ca Yehova pa nyengo yace yoikidwa, pakati pa ana a Israyeli?

8 Ndipo Mose ananena nao, Baimani; ndimve couza Yehova za inu.

9 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

10 Nena ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Angakhale munthu wa inu kapena wa mibadwo yanu, adetsedwa, cifukwa ca mtembo, kapena pokhala paulendo, koma azicitira Yehova Paskha.

11 Mwezi waciwiri, tsiku lace lakhumi ndi cinai, madzulo, aucite; audye ndi mkate wopanda cotupitsa ndi msuzi wowawa.

12 Asasiyeko kufikira m'mawa, kapena kuthyolapo pfupa; aucite monga mwa lemba lonse la Paskha.

13 Munthu akakhala woyera, wosakhala paulendo, koma akaleka kucita Paskha, amsadze munthuyo kwa anthu a mtundu wace; popeza sanabwera naco copereka ca Yehova pa nyengo yace yoikidwa, munthuyu asenze kucimwa kwace.

14 Ndipo mlendo akakhala mwa inu, nakacitira Yehova Paskha, azicita monga mwa lemba la Paskha, ndi monga mwa ciweruzo cace; lemba likhale limodzi kwa inu, ndi kwa mlendo, ndi kwa wobadwa m'dziko.

15 Ndipo tsiku loutsa kacisi mtambo unaphimba kacisi, ndiwo cihema cokomanako; ndipo madzulo padaoneka pakacisi ngati moto, kufikira m'mawa.

16 Kudatero kosalekeza; mtambo umaciphimba, ndimoto umaoneka usiku,

17 Ndipo pokwera mtambo kucokera kucihema, utatero ana a Israyeli amayenda ulendo wao; ndipo pamalo pokhala mtambo, pamenepo ana a Israyeli amamanga mahema ao.

18 Pakuwauza Yehova ana a Israyeli amayenda ulendo, powauza Yehova amamanga mahema ao; masiku onse mtambo ukakhala pamwamba pa kacisi amakhala m'cigono.

19 Ndipo pakukhalitsa mtambo masiku ambiri pamwamba pa kacisi, pamenepo ana a Israyeli anasunga udikiro wa Yehova osayenda ulendo.

20 Ndipo pokhala mtambo pamwamba pa kacisi masiku pang'ono; pamenepo anakhala m'cigono monga awauza Yehova, nayendanso ulendo monga anauza Yehova.

21 Koma mtambo ukakhala kuyambira madzulo kufikira m'mawa; pokwera mtambo m'mawa, ayenda ulendo; ngakhale msana ngakhale usiku, pokwera mtambo, ayenda ulendo.

22 Ngakhale masiku awiri, kapena mwezi, kapena masiku ambiri, pokhalitsa mtambo pamwamba pa kacisi ndi kukhalapo, ana a Israyeli anakhala m'cigono, osayenda ulendo; koma pakukwera uwu, anayenda ulendo.

23 Powauza Yehova amanga mahema, powauza Yehova ayenda ulendo; anasunga udikiro wa Yehova powauza Yehova mwa dzanja la Mose.

10

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Dzipangire malipenga awiri asiliva; uwasule mapangidwe ace; ucite nao poitana khamu, ndi poyendetsa a m'zigono.

3 Akaliza, khamu lonse lisonkhane kuli iwe ku khomo la cihema cokomanako,

4 Akaliza limodzi, pamenepo akalonga, akuru a zikwi a m'Israyeli, azisonkhana kuli iwe.

5 Mukaliza cokweza, ayende a m'zigono za kum'mawa.

6 Mukalizanso cokweza, a m'zigono za kumwela ayende; alize cokweza pakumuka.

7 Pomemeza msonkhano mulize, wosati cokweza ai.

8 Ana amuna a Aroni, ansembe, ndiwo aziliza malipenga; ndipo akhale kwa inu lemba losatha ku mibadwo yanu.

9 Ndipo pamene mupita kunkhondo m'dziko lanu kucita nkhondo pa mdani wakusautsa inu, mulize cokweza ndi malipenga; ndipo Yehova Mulungu wanu adzakumbukila inu, nadzakupulumutsani kwa adani anu.

10 Momwemo tsiku lakukondwera inu, ndi nyengo zoikidwa zanu, ndi poyamba miyezi yanu, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza, ndi pa nsembe zanu zoyamika; ndipo akhale kwa inu cikumbutso pamaso pa Mulungu wanu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

11 Ndipo kunacitika, caka caciwiri, mwezi waciwiri, tsiku la makumi awiri la mweziwo, kuti mtambo unakwera kucokera kwa kacisi wa mboni.

12 Ndipo ana a Israyeli anayenda monga mwa maulendo ao, kucokera m'cipululu ca Sinai; ndi mtambo unakhala m'cipululu ca Parana.

13 Potero anayamba ulendo wao monga mwa mau a Yehova ndi dzanja la Mose.

14 Ndipo anayamba kuyenda a mbendera ya cigono ca ana a Yuda monga mwa magulu ao; woyang'anira gulu lace ndiye Nahesoni mwana wa Aminadabu.

15 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Isakara panali Netaneli mwana wa Zuwara.

16 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Zebuloni panali Eliyabu mwana wa Heloni.

17 Ndipo anagwetsa kacisi; ndi ana a Gerisoni, ndi ana a Merari, akunyamula kacisi, anamuka naye.

18 Ndi a mbendera ya cigono ca Rubeni, anayenda monga mwa magulu ao; ndipo pa gulu lace anayang'anira Elizuri mwana wa Sedeuri.

19 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Simeoni anayang'anira Selumiyeli mwana wa Zurisadai.

20 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Gadi anayang'anira Eliyasafe mwana wa Deyueli.

21 Pamenepo Akohati anayenda, ndi kunyamula zopatulika, ndi enawo anautsiratu kacisi asanafike iwowa.

22 Ndipo anayenda a mbendera ya cigono ca ana a Efraimu, monga mwa magulu ao; ndi pa gulu lace anayang'anira Elizama mwana wa Amihudi.

23 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Manase anayang'anira Gamaliyeli mwana wa Pedazuri.

24 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Benjamini anayang'anira Abidana mwana wa Gideoni.

25 Pamenepo anayenda a mbendera ya cigono ca ana a Dani, ndiwo a m'mbuyombuyo a zigono zonse, monga mwa magulu ao; ndi pa gulu lace anayang'anira Ahiyezeri mwana wa Amisadai.

26 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Aseri anayang'anira Pagiyeli mwana wa Okirani.

27 Ndi pa gulu la pfuko la ana a Nafitali anayang'anira Ahira mwana wa Enani.

28 Potero maulendo a ana a Israyeli anakhala monga mwa magulu ao; nayenda ulendowao.

29 Ndipo Mose anati kwa Hobabu mwana wa Reueli Mmidyani mpongozi wa Mose, Ife tirikuyenda kumka ku malo amene Yehova anati, Ndidzakupatsani awa; umuke nafe, tidzakucitira zokoma; popeza Yehova wanenera Israyeli zokoma.

30 Koma anati kwa iye, Sindidzamuka nanu; koma ndipita ku dziko langa, ndi kwa abale anga.

31 Koma anati, Usatisiyetu; popeza udziwa poyenera kumanga ife m'cipululu, ndipo udzakhala maso athu.

32 Ndipo kudzatero, ukamuka nafe, inde, kudzali kuti zokoma ziri zonse Yehova aticitira ife, zomwezo tidzakucitira iwe.

33 Ndipo anayenda kucokera ku phiri la Yehova ulendo wa masiku atatu; ndipo likasa la cipangano ca Yehova, linawatsogolera ulendo wa masiku atatu kuwafunira popumulira.

34 Ndipo mtambo wa Yehova unali pamwamba pao msana, pakuyenda iwo kucokera kucigono.

35 Ndipo kunali pakucoka kumka nalo likasa, Mose anati, Ukani Yehova, abalalike adani anu; akuda Inu athawe pamaso panu.

36 Ndi pakupumula ili anati, Bwerani Yehova kwa zikwi zikwi za Israyeli.

11

1 Ndipo anthu anaipa, namadandaula m'makutu a Yehova; ndipo pamene Yehova anamva anapsa mtima; ndi mota wa Yehova unayaka pakati pao, nunyeketsa ku cilekezero ca cigono.

2 Pamenepo anthu anapfuulira kwa Mose; ndi Mose anapemphera kwa Yehova, ndi motowo unazimika.

3 Ndipo anacha malowo dzina lace Tabera; popeza moto wa Yehova udayaka pakati pao.

4 Ndipo anthu osokonezeka ali pakati pao anagwidwa naco cilakolako; ndi ana a Israyeli omwe analiranso, nati, Adzatipatsa nyama ndani?

5 Tikumbukira nsomba tinazidya m'Aigupto cabe, mankaka, ndi mavwendi, ndi anyesi a mitundu itatu;

6 koma tsopano moyo wathu waphwa; tiribe kanthu pamaso pathu koma mana awa.

7 Ndipo mana ananga zipatso zampasa, ndi maonekedwe ace ngati maonekedwe a bedola.

8 Anthu amamka, nawaola, nawapera ndi mphero, kapena kuwasinja mumtondo, nawaphika m'mphika, nawaumba timitanda; ndi powalawa anali ngati timitanda tokazinga ndi mafuta.

9 Ndipo pakugwa mame pacigono usiku, mana anagwapo.

10 Ndipo Mose anamva anthu alikulira m'mabanja ao, yense pakhomo pa hema wace; ndipo Yehova anapsa mtima ndithu, ndipo kudamuipira Mose.

11 Ndipo Mose anati kwa Yehova, Munacitiranji coipa mtumiki wanu? ndalekeranii kupeza ufulu pamaso panu, kuti muika pa ine katundu wa anthu awa onse?

12 Kodi ndinaima nao anthu awa onse? kodi ndinawabala, kuti munene nane, Uwayangate ngati mlezi afukata khanda, kumka nao ku dzikolo mudalumbirira makolo ao?

13 Ndidzaiona kuti nyama yakuwapatsa anthu awa onse? pakuti amalirira ine, ndi kuti, Tipatseni nyama, tidye.

14 Sinditha kuwasenza anthu awa onse ndekha, pakuti andilemera ine.

15 Ndipo ngati mundicitira cotero, mundiphetu tsopano apa, ngati ndapeza ufulu pamaso panu, ndisayang'ane tsoka langa.

16 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Undisonkhanitsire amuna makumi asanu ndi awiri mwa akuru a Israyeli, amene uwadziwa kuti ndiwo akuru a anthu, ndi akapitao ao; nubwere nao ku cihema cokomanako, kuti aimeko pamodzi ndi iwe.

17 Pamenepo ndidzatsika ndi kulankhula nawe komweko; ndipo ndidzatengako mzimu uti pa iwe, ndi kuika pa iwowa; adzakuthandiza kusenza katundu wa anthu awa, kuti usasenze wekha.

18 Ndipo unene ndi anthu, Mudzipatuliretu, mawa mudzadya nyama; popeza mwalira m'makutu a Yehova, ndi kuti, Adzatipatsa nyama ndani? popeza tinakhala bwino m'Aigupto, Potero Yehova adzakupatsani nyama, ndipo mudzadya.

19 Simudzadya tsiku limodzi, kapena masiku awiri, kapena masiku asanu, kapena masiku khumi, kapena masiku makumi awiri;

20 koma mwezi wamphumphu, kufikira ibwera m'mphuno mwako, ndi kuti ufukidwa nayo, pakuti mwakaniza Yehova wakukhala pakati pa inu, ndi kulira pamaso pace, ndi kuti, Tinaturukiranji m'Aigupto?

21 Ndipo Mose anati, Anthu amene ndiri pakati pao, ndiwo zikwi mazana asanu ndi limodzi oyenda pansi, ndipo Inu mwanena, Ndidzawapatsa nyama, kuti adye mwezi wamphumphu.

22 Kodi adzawaphera magulu a nkhosa ndi ng'ombe, kuwakwanira? kapena kodi nsomba zonse za m'nyanja zidzawasonkhanira pamodzi, kuwakwanira?

23 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Kodi dzanja la Mulungu lafupikira? tsopano udzapenya ngati mau anga adzakucitikira kapena iai.

24 Ndipo Mose anaturuka, nauza anthu mau a Yehova; nasonkhanitsa akuru a anthu makumi asanu ndi awiri, nawaimika pozungulira pa cihema.

25 Ndipo Yehova anatsika mumtambo, nanena nave, natengako mzimu uli pa iye, nauika pa akuru makumi asanu ndi awiri; ndipo kunali kuti pokhala mzimu pa iwowa, ananenera; koma osabwerezanso.

26 Koma amuna awiri anatsalira m'cigono, dzina la wina ndiye Elidadi, dzina la mnzace ndiye Medadi; ndipo mzimuwo unakhala pa iwo; iwo ndiwo mwa oitanidwawo, koma sanaturuka kumka kucihema; ndipo ananenera m'cigono.

27 Ndipo anathamanga anyamata, nauza Mose, nati, Elidadi ndi Medadi alikunenera m'cigono.

28 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose kuyambira ubwana wace, anayankha nati, Mose, mfumu yanga, aletseni.

29 Koma Mose anati kwa iye, Kodi ucita nsanje nao cifukwa ca ine? Mwenzi anthu onse a Yehova atakhala aneneri! mwenzi Yehova atawaikira mzimu wace!

30 Ndipo Mose ndi akulu onse a Israyeli anasonkhana kucigono.

31 Ndipo kudacokera mphepo kwa Yehova, nidza nazo zinziri zocokera kunyanja, nizitula kucigono, ulendo wa tsiku limodzi dera lino, ndi ulendo wa tsiku limodzi dera lina, pozungulira pa cigono, ndipo zinabisa nthaka ngati muyeso wa mikono iwiri.

32 Ndipo anthu anauka tsiku lonselo, ndi usiku wace wonse, ndi mawa lace lonse, nakusa zinzirizo; wokusa pang'ono anakusa zodzaza mahomeri khumi; ndipo anadziyanikira izi pozungulira pa cigono.

33 Nyamayi ikali pakati pa mano, asanaitafune, Mulungu anapsa mtima pa anthuwa, ndipo Yehova anawakantha anthu ndi kukantha kwakukuru ndithu.

34 Ndipo anacha malowo dzina lace Kibiroti Hatava; popeza pamenepo anaika anthu osusuka.

35 Kucokera ku Kibiroti Hatava anthuwo anayenda kumka ku Hazeroti; nakhala ku Hazeroti.

12

1 Ndipo Miriamu ndi Aroni anatsutsana naye Mose cifukwa ca mkazi mtundu wace Mkusi amene adamtenga; popeza adatenga mkazi Mkusi.

2 Ndipo anati, Kodi Yehova wanena ndi Mose yekha? sananenanso ndi ife nanga? Ndipo Yehova anamva.

3 Koma munthuyu Mose ndiye wofatsa woposa anthu onse a pa dziko lapansi.

4 Ndipo Yehova anati kwa Mose, ndi Aroni, ndi Miriamu modzidzimutsa, Turukani inu atatu kudza ku cihema cokomanako. Pamenepo anaturuka atatuwo.

5 Ndipo Yehova anatsika mumtambo njo, naima pa khomo la cihema, naitana Aroni ndi Miriamu; naturuka onse awiri.

6 Ndipo anati, Tamvani tsono mau anga; pakakhala mneneri pakati pa inu, Ine Yehova ndidzizindikiritsa kwa iye m'masomphenya, ndinena naye m'kulota.

7 Satero mtumiki wanga Mose; ndiye wokhulupirika m'nyumba mwanga monse.

8 Ndimanena naye pakamwa ndi pakamwa, maonekera, osati mophiphiritsa; ndipo amapenyerera maonekedwe a Yehova; potero munalekeranji kuopa kutsutsana naye mtumiki wanga, Mose.

9 Pamenepo Mulungu anawapsera mtima iwo; nawacokera iye.

10 Ndipo mtambo unacoka pacihema; ndipo taonani, Miriamu anali wakhate, wa mbu ngati cipale cofewa; ndipo Aroni anapenya Miriamu, taonani, anali wakhate.

11 Ndipo Aroni anati kwa Mose, Mfumu yanga, musatiikiretu kucimwa kumene tapusa nako, ndi kucimwa nako.

12 Asakhaletu iye ngati wakufa, amene dera lina la mnofu wace watha poturuka iye m'mimba mwa mace.

13 Ndipo Mose anapfuulira kwa Yehova, ndi kuti, Mciritsenitu, Mulungu,

14 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Atate wace akadamlabvulira malobvu pankhope pace sakadacita manyazi masiku asanu ndi awiri? ambindikiritse kunja kwa cigono masiku asanu ndi awiri; ndipo atatero amlandirenso.

15 Pamenepo anambindikiritsa Miriamu kunja kwa cigono masiku asanu ndi awiri; ndipo anthu sanayenda ulendo kufikira atamlandiranso Miriamu.

16 Ndipo atatero anthuwo anamka ulendo wao kucokera ku Hazeroti, namanga mahema ao m'cipululu ca Parana.

13

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Udzitumire amuna, kuti azonde dziko la Kanani, limene ndirikupatsa ana a Israyeli; utumize munthu mmodzi wa pfuko liri lonse la makolo ao, yense kalonga pakati pa anzace.

3 Ndipo Mose anawatumiza kucokera ku cipululu ca Parana monga mwa mau a Yehova; amuna onsewa ndiwo akuru a ana a Israyeli.

4 Maina ao ndi awa: wa pfuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri.

5 Wa pfuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori.

6 Wa pfuko la Yuda, Kalebi mwana wa Yefune.

7 Wa pfuko la Isakara, Igali mwana wa Yosefe.

8 Wa pfuko la Efraimu, Hoseya mwana wa Nuni.

9 Wa pfuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu.

10 Wa pfuko la Zebuloni, Gadiyeli mwana wa Sodi.

11 Wa pfuko la Yosefe, wa pfuko la Manase, Gadi mwana wa Susi.

12 Wa pfuko la Dani, Amiyeli mwana wa Gemali.

13 Wa pfuko la Aseri, Setri mwana wa Mikayeli.

14 Wa pfuko la Nafitali, Nabi mwana wa Vopisi.

15 Wa pfuko la Gadi, Geyuelimwana wa Maki.

16 Awandi maina a amunawo Mose anawatumira azonde dziko. Ndipo Mose anamucha Hoseya mwana wa Nuni Yoswa.

17 Potero Mose anawatuma azonde dziko la Kanani, nanena nao, Kwerani uko kumwela, nimukwere kumapiri;

18 mukaone dziko umo liriri; ndi anthu akukhala m'mwemo, ngati ali amphamvu kapena ofok a, ngati acepa kapena acuruka;

19 ndi umo liriri dzikoli lokhalamo iwo, ngati lokoma, kapena loipa; ndi umo iriri midziyo akhalamo iwo, ngati akhala poyera kapena m'malinga;

20 ndi umo iriri nthaka, ngati yopatsa, kapena yosuka, ngati pali mitengo, kapena palibe, Ndipo limbikani mtima, nimubwere nazo zipatso za m'dzikomo. Koma nyengoyi ndiyo nyengo yoyamba kupsa mphesa.

21 Pamenepo anakwerako, nazonda dziko kuyambira cipululu ca Zini kufikira Rehobo, polowa ku Hamati.

22 Ndipo anakwera njira ya kumwela nafika ku Hebroni; ndi apa panali Ahimani, Sesai, ndi Talmai, ana a Anaki. (Koma atamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri ndipo anamanga Zoani m'Aigupto.)

23 Ndipo anadza ku cigwa ca Esikolo, nacekako tsango limodzi la mphesa, nalisenza awiri mopika; anabwera nazonso makangaza ndi nkhuyu.

24 Malowa anawacha cigwa ca Esikolo, cifukwa ca tsangolo ana a lsrayeli analicekako.

25 Pamenepo anabwerera atazonda dziko, atatha masiku makumi anai.

26 Ndipo anamuka, nadza kwa Mose, ndi Aroni, ndi khamu lonse la ana a Israyeli, ku cipululu ca Parana ku Kadesi; ndipo anabwezera mau iwowa, ndi khamu lonse, nawaonetsa zipatso za dzikoli.

27 Ndipo anafotokozera, nati, Tinakafika ku dziko limene munatitumirako, ndilo ndithu a moyenda mkaka ndi uci ngati madzi; ndi zipatso zace siizi.

28 Komatu anthu okhala m'dzikomo ngamphamvu; ndi midziyo nja malinga, yaikuru ndithu: ndipo tinaonakonso ana a Anaki.

29 Aamaleke akhala m'dziko la kumwera; ndi Ahiti, ndi Ayebusi, ndi Aamori, akhala ku mapiri, ndi Akanani akhala kunyanja, ndi m'mphepete mwa Yordano.

30 Koma Kalebi anatontholetsa anthu pamaso pa Mose, nati, Tikwere ndithu ndi kulilandira lathu lathu; popeza tikhozadi kucita kumene.

31 Koma anthu adakwera nayewo anati, Sitikhoza kuwakwerera anthuwo; popeza atiposa mphamvu,

32 Ndipo anaipsira ana a Israyeli mbiri ya dziko adalizonda, nati, Dzikoli tapitamo kulizonda, ndilo dziko lakutheramo anthu okhalamo; ndi anthu onse tidaona pakati pace ndiwo anthu atali misinkhu.

33 Tinaonakonso Anefili, ana a Anaki, obadwa ndi Anefili; ndipo tinaoneka m'maso mwathu ngati zinsidzi; momwemonso tinaoneka m'maso mwao.

14

1 Pamenepo khamu lonse linakweza mau ao, napfuula; ndipo anthuwo analira usikuwo.

2 Ndipo ana onse a Israyeli anadandaulira Mose ndi Aroni; ndi khamu lonse linanena nao, Mwenzi tikadafa m'dziko la Aigupto; kapena mwenzi tikadafa m'cipululu muno!

3 Ndipo Yehova atitengeranii kudza nafe kudziko kuno, kuti tigwe nalo lupanga? Akazi athu ndi makanda athu adzakhala cakudya cao; kodi sikuli bwino tibwerere ku Aigupto?

4 Ndipo anati wina ndi mnzace, Tiike mtsogoleri, tibwerere ku Aigupto.

5 Pamenepo Mose ndi Aroni anagwa nkhope pansi pamaso pa msonkhano wonse wa khamu la ana a Israyeli.

6 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, ndi Kalebi mwana wa Yefune, ndiwo a iwo aja adazonda dzikolo, anang'amba zobvala zao;

7 nanena ndi khamu lonse la ana a Israyeli, nati, Dziko tapitamo kulizonda, ndilo dziko lokometsetsa ndithu.

8 Yehova akakondwera nafe, adzatilowetsa m'dzikomo, ndi kutipatsa ilo; ndilo dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi.

9 Cokhaci musamapikisana naye Yehova, musamaopa anthu a m'dzikomo; pakuti ndiwo mkate wathu; mthunzi wao wawacokera, ndipo Yehova ali nafe; musamawaopa.

10 Koma khamu lonse lidati liwaponye miyala, Ndipo ulemerero wa Yehova unaoneka m'cihema cokomanako kwa ana onse a Israyeli.

11 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Anthu awa adzaleka liti kundinyoza? ndipo adzayamba liti kundikhulupirira, cinkana zizindikilo zonse ndinazicita pakati pao?

12 Ndidzawakantha ndi mliri, ndi kuwacotsera colowa cao, ndipo ndidzakusandutsa iwe mtundu wa anthu waukuru ndi wamphamvu koposa iwowa.

13 Ndipo Mose anati kwa Yehova, Pamenepo Aaigupto adzamva; popeza munakweza anthu awa ndi mphamvu yanu kuwacotsa pakati pao;

14 ndipo adzawauza okhala m'dziko muno; adamva kuti inu Yehova muli pakati pa anthu awa; pakuti muoneka mopenyana, Yehova, ndi mtambo wanu umaima pamwamba pao, ndipo muwatsogolera, ndi mtambo njo msana, ndi moto njo usiku.

15 Ndipo mukapha anthu awa ngati munthu mmodzi, pamenepo amitundu amene adamva mbiri yanu adzanena, ndi kuti,

16 Popeza Yehova sanakhoza kuwalowetsa anthu awa m'dziko limene anawalumbirira, cifukwa cace anawapha m'cipululu.

17 Ndipo tsopano, ikuletu mphamvu ya Mbuye wanga, monga mudanena, ndi kuti,

18 Yehova ndiye wolekereza, ndi wa cifundo cocuruka, wokhululukira mphulupulu ndi kulakwa, koma wosamasula woparamula; wakuwalanga ana cifukwa ca mphulupulu ya atate ao, kufikira mbadwo wacitatu ndi wacinai.

19 Khululukiranitu mphulupulu ya anthu awa, monga mwa cifundo canu cacikuru, ndi monga mudalekerera anthu awa, kuyambira Aigupto kufikira tsopano.

20 Ndipo Yehova anati, Ndakhululukira monga mwa mau ako:

21 koma ndithu, pali Ine, dziko lonse lapansi lidzadzazidwa ndi ulemerero wa Yehova;

22 popeza anthu onse awa amene adaona ulemerero wanga, ndi zizindikilo zanga, ndidazicita m'Aigupto ndi m'cipululu, koma anandiyesa Ine kakhumi aka, osamvera mau anga;

23 sadzaona dzikoli ndidalumbirira makolo ao, ngakhale mmodzi wa iwo akundinyoza Ine, sadzaliona;

24 koma mtumiki wanga Kalebi, popeza anali nao mzimu wina, nanditsata monsemo, ndidzamlowetsa iyeyu m'dziko muja analowamo; ndi mbeu zace zidzakhala nalo.

25 Koma Aamaleki ndi Akanani akhala m'cigwamo; tembenukani mawa, nimumke ulendo wanu kucipululu, njira ya ku Nyanja Yofiira.

26 Ndipo Yehova ananena kwa Mose ndi Aroni, nati,

27 Ndileke khamu loipa ili lakudandaula pa Ine kufikira liti? Ndidamva madandaulo a ana a Israyeli, amene amandidandaulira.

28 Nunene nao, Pali Ine, ati Yehova, ndidzacitira inu ndithu monga mwanena m'makutu mwanga;

29 mitembo yanu idzagwa m'cipululu muno; ndi owerengedwa anu onse, monga mwa kuwerenga kwanu konse, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, akudandaula pa Ine;

30 simudzalowa inu m'dzikolo, ndinakwezapo dzanja langa kukukhalitsani m'mwemo, koma Kalebi mwana wa Yefune, ndi Yoswa mwana wa Nuni ndiwo.

31 Koma makanda anu, amene munanena za iwowa kuti adzakhala cakudya, amenewo ndidzavalowetsa, ndipo adzadziwa dzikolo mudalikana.

32 Koma inu, mitembo yanu idzagwa m'cipululu muno.

33 Ndipo ana anu adzakhala oyendayenda m'cipululu zaka makumi anai, nadzasenza kupulukira kwanu, kufikira mitembo yanu yatha m'cipululu.

34 Monga mwa kuwerenga kwa masiku amene munazonda dziko, masiku makumi anai, tsiku limodzi kuwerenga caka cimodzi, mudzasenza mphulupulu zanu, zaka makumi anai, ndipo mudzadziwa kuti ndaleka lonjezano langa.

35 Ine Yehova ndanena, ndidzacitira ndithu ici khamu ili lonse loipa lakusonkhana kutsutsana nane; adzatha m'cipululu muno, nadzafamo.

36 Ndipo amunawo, amene Mose anawatumiza kukazonda dziko, amene anabwera nadandaulitsa khamu lonse pa iye, poipsa mbiri ya dziko,

37 amuna amene anaipsa mbiri ya dziko, anafa ndi mliri pamaso pa Yehova.

38 Koma Yoswa mwana wa Nuni, ndi Kalebi mwana wa Yefune, anakhala ndi moyo mwa amuna aja adamukawo kukazonda dziko.

39 Ndipo Mose anauza ana a Israyeli mao onse awa; ndipo anthu anamva cisoni cambiri.

40 Ndipo anauka mamawa, nakwera pamwamba pa, phiri, nati, Tiri pano, tidzakwera kumka ku malo amene Yehova ananena; popeza tacimwa.

41 Ndipo Mose anati, Mutero cifukwa ninji kulakwira mau a Yehova, popeza simudzapindula nako?

42 Musakwereko, pakuti Yehova sali pakati pa inu; kuti angakukantheni adani anu.

43 Pakuti Aamaleki ndi Akanani ali komweko patsogolo panu, ndipo mudzagwa ndi lupanga; popeza mwabwerera m'mbuyo osatsata Yehova, cifukwa cace Yehova sadzakhala nanu.

44 Koma anakwera pamwamba pa phiri modzikuza; koma likasa la cipangano la Yehova, ndi Mose, sanacoka kucigono.

45 Pamenepo anatsika Aamaleki, ndi Akanani, akukhala m'phirimo nawakantha, nawapha kufikira ku Horima.

15

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose nati,

2 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mukakalowa m'dziko lokakhalamo inu, limene ndirikupatsa inu,

3 ndipo mukakonzera Yehova nsembe yamoto, nsembe yopsereza, kapena yophera, pocita cowinda ca padera, kapena nsembe yaufulu, kapena nsembe ya pa nyengo zanu zoikika, kumcitira Yehova pfungo lokoma, la ng'ombe kapena nkhosa;

4 pamenepo iye wobwera naco copereka cace kwa Yehova, azibwera nayo nsembe yaufa, limodzi la magawo khumi la ufa wosalala, wosanganiza ndi limodzi la magawo anai la bini la mafuta;

5 ndipo uzikonzera nsembe yopsereza kapena yophera, vinyo wa nsembe yothira, limodzi la magawo anai la bini, ukhale wa mwana wa nkhosa mmodzi.

6 Kapena ukonzere nkhosa yamphongo nsembe yaufa, awiri mwa magawo khumi a ufa wosalala, wosanganiza ndi mafuta, limodzi la magawo atatu la bini.

7 Ndipo ubwere naye vinyo wa nsembe yothira, limodzi la magawo atatu la bini, acitire Yehova pfungo lokoma.

8 Ndipo pamene mukonza ng'ombe ikhale nsembe yopsereza, kapena yophera, kucita cowinda ca padera, kapena ikhale nsembe yoyamika ya Yehova;

9 abwere nayo, pamodzi ndi ng'ombeyo, nsembe ya ufa wosalala, atatu mwa magawo khumi wosanganiza ndi mafuta, limodzi la magawo awiri la bini.

10 Ndipo ubwere naye vinyo wa nsembe yothira limodzi la magawo awiri la hini, ndiye nsembe yamoto ya pfungo: lokoma, ya Yehova.

11 Kudzatero ndi ng'ombe iri yonse, kapena nkhosa yamphongo iri yonse, kapena mwana wa nkhosa ali yense, kapena mwana wa mbuzi ali yense.

12 Monga mwa kuwerenga kwace kwa izi muzikonza, muzitero ndi yonse monga mwa kuwerenga kwace.

13 Onse akubadwa m'dzikomo acite izi momwemo, pobwera nayo kwa Yehova nsembe yamoto ya pfungo lokoma.

14 Ndipo akakhala nanu mlendo, kapena ali yense wakukhala pakati pa inu mwa mibadwo yanu, nakacitira Yehova nsembe yamoto ya pfungo lokoma; monga mucita inu, momwemo iyenso,

15 Kunena za khamu, pakhale lemba limodzi kwa inu, ndi kwa mlendo wakukhala kwanu, ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu; monga mukhala inu, momwemo mlendo pamaso pa Yehova.

16 Pakhale cilamulo cimodzi ndi ciweruzo cimodzi kwa inu ndi kwa mlendo wakukhala kwanu.

17 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

18 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Pamene mulowa m'dziko limene ndirikukulowetsani,

19 kudzali, pakudya inu mkate wa m'dzikolo, muzikwezera Yehova nsembe yokweza.

20 Pa mtanda wanu woyamba muperekeko kamtanda, kakhale nsembe yokweza; monga mumacitira nsembe yokweza ya popuntha tirigu, momwemo muzikakweza.

21 Muzipatsa Yehova nsembe yokweza yoitenga ku mtanda wanu woyamba, mwa mibadwo yanu.

22 Ndipo pamene mulakwa, osacita mau awa onse amene Yehova ananena ndi Mose;

23 ndizo zonse Yehova anakuuzani ndi dzanja la Mose, kuyambira tsikulo Yehova anauza, ndi kunkabe m'mibadwo yanu;

24 pamenepo kudzali, ngati anacicita osati dala, osacidziwa khamulo, khamu lonse lipereke ng'ombe yamphongo ikhale nsembe yopsereza, ya pfungo lokoma ya Yehova, pamodzi ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe yace yothira, monga mwa ciweruzo cace; ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo.

25 Ndipo wansembe azicita cotetezera khamu lonse la ana a Israyeli, ndipo adzakhululukidwa; popeza sanacita dala, ndipo anadza naco copereka cao, nsembe yamoto kwa Yehova, ndi nsembe yao yaucimo pamaso pa Yehova, cifukwa ca kulakwa osati dala.

26 Ndipo khamu lonse la ana a Israyeli, adzakhululukidwa, ndi mlendo yemwe wakukhala pakati pao; popeza khamu lonse linacicita osati dala.

27 Ndipo akacimwa munthu mmodzi osati dala, abwere nayo mbuzi yamsoti ya caka cimodzi, ikhale nsembe yaucimo.

28 Ndipo wansembe acite comtetezera munthu wakulakwa, osalakwa dala pamaso pa Yehova, kumcita comtetezeraj ndipo adzakhululukidwa.

29 Kunena za wobadwa m'dziko mwa ana a Israyeli, ndi mlendo wakukhala pakati pao, mukhale naco cilamulo cimodzi kwa iye wakucita kanthu kosati dala.

30 Koma munthu wakucita kanthu dala, ngakhale wobadwa m'dziko kapena mlendo, yemweyo acitira Yehova mwano; ndipo munthuyo amsadze pakati pa anthu a mtundu wace.

31 Popeza ananyoza mau a Yehova, nathyola lamulo lace; munthuyu amsadze konse; mphulupulu yace ikhale pa iye.

32 Ndipo pokhala ana a Israyeli m'cipululu, anapeza munthu wakufuna nkhuni tsiku la Sabata.

33 Ndipo amene adampezawo alinkufuna nkhuni anabwera naye kwa Mose ndi Aroni, ndi kwa khamu lonse.

34 Ndipo anathanga wamsunga, popeza sicinanenedwa coyenera kumcitira iye.

35 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Amuphe munthuyu ndithu; khamu lonse limponye miyala kunja kwa cigono.

36 Pamenepo khamu lonse linamturutsa kunja kwa cigono, ndi kumponya miyala, ndipo anafa; monga Yehova adauza Mose.

37 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

38 Nena ndi ana a Israyeli, nuwauze kuti adziombere mphonje m'mphepete mwa zobvala zao, mwa mibadwo yao, naike pamphonje m'mphepetemo thonje lamadzi.

39 Ndipo cikhale kwa inu mphonje, yakuti muziyang'anirako, ndi kukumbukila malamulo onse a Yehova, ndi kuwacita, ndi kuti musamazondazonda kutsata za m'mtima mwanu, ndi za m'maso mwanu zimene mumatsata ndi cigololo;

40 kuti mukumbukile ndi kucita malamulo anga onse, ndi kukhala wopatulikira Mulungu wanu.

41 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, wakukuturutsani m'dziko la Aigupto, kuti ndikhale Mulungu wanu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

16

1 Koma Kora, mwana wa Izara, mwana wa Kohati, mwana wa Levi, anatenga Datani ndi Abiramu, ana a Eliyabu, ndi Oni mwana wa Peleti, ana a Rubeni;

2 ndipo anauka pamaso pa Mose, pamodzi ndi amuna: mazana awiri mphambu makumi asanu a ana a Israyeli, ndiwo akalonga a khamulo, oitanidwa a msonkhano, amuna omveka.

3 Ndipo anasonkhana motsutsana pa Mose ndi Aroni, nanena nao, Mukula mphamvu inu, pakuti khamu lonse nlopatulika, onsewa, ndipo Yehova ali pakati pao; mudzikuza bwanji pa msonkhano wa Yehova?

4 Pamene Mose anamva ici anagwa nkhope yace pansi;

5 nanena ndi Kora ndi khamu lace lonse, ndi kuti, M'mawa Yehova adzatizindikiritsa anthu ace ndi ayani, wopatulika ndani, amene adzamsendeza pafupi pa iye; ndi iye amene anamsankha adzamsendeza pafupi pa iye.

6 Citani ici; dzitengereni mbale za zofukiza, Kora, ndi khamu lace lonse;

7 nimuikemo moto, muikenso cofukiza pamenepo, pamaso pa Yehova, mawa; ndipo kudzali kuti amene Yehova amsankha, wopatulika ndiye; mwakula mphamvu, inu ana a Levi.

8 Ndipo Mose ananena ndi Kora, Tamvani tsono, inu ana a Levi;

9 kodi muciyesa cinthu cacing'ono, kuti Mulungu wa Israyeli anakusiyanitsani ku khamu la Israyeli, kukusendezani pafupi pa iye, kucita nchito ya kacisi wa Yehova, ndi kuima pamaso pa khamu kuwatumikira;

10 ndi kuti anakusendeza iwe, ndi abale ako onse, ana a Levi, pamodzi ndi iwe? ndipo kodi mufunanso nchito ya nsembe?

11 Cifukwa cace, iwe ndi khamu lonse mwasonkhana kutsutsana ndi Yehova; ndipo Aroniyo ndani, kuti mudandaule pa iye?

12 Ndipo Mose anatuma kukaitaniza Datani ndi Abiramu, ana a Eliyabu; koma anati, Sitifikako:

13 kodi ndi cinthu cacing'ono kuti watikweza kuticotsa m'dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi, kutipha m'cipululu; koma udziyesanso ndithu kalonga wa ife?

14 Ndiponso sunatilowetsa m'dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi, kapena kutipatsa colowa ca minda, ndi minda yamphesa; kodi udzakolowola amuna awa maso ao? Sitifikako.

15 Pamenepo Mose adapsa mtima, ndipo anati kwa Yehova, Musasamalira copereka cao; siodinalanda buru wao mmodzi, kapena kucitira coipa mmodzi wa iwowa.

16 Ndipo Mose anati kwa Kora, Iwe ndi khamu lako lonse mukhale pamaso pa Yehova mawa, iwe ndi iwowa, ndi Aroni;

17 nimutenge munthu yense mbale yace yofukizamo, nimuike cofukiza m'mwemo, nimubwere nazo, yense mbale yace yofukizamo pamaso pa Yehova, mbale zofukizamo mazana awiri ndi makumi asanu; ndi iwe, ndi Aroni, yense mbale yace yofukizamo.

18 Potero munthu yense anatenga mbale yace yofukizamo, naikamo moto, naikapo cofukiza, naima pa khomo la cihema cokomanako pamodzi ndi Mose ndi Aroni.

19 Ndipo Kora anasonkhanitsa khamu lonse mopikisana nao ku khomo la cihema cokomanako; ndipo ulemerero wa Yehova unaoneka kwa khamu lonse.

20 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,

21 Dzipatu, leni pakati pa khamu lino, kuti ndi wathe m'kamphindi.

22 Ndipo anagwa nkhope zao pansi, nati, Mulungu, ndinu Mulungu wa mizimu ya anthu onse, walakwa munthu mmodzi, ndipo kodi mukwiya nalo khamu lonse?

23 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

24 Nena ndi khamulo, ndi kuti, Kwerani kucoka pozungulira mahema a Kora, Datani, ndi Abiramu.

25 Ndipo Mose anauka namuka kwa Datani ndi Abiramu; ndi akuru a Israyeli anamtsata.

26 Ndipo ananena ndi khamulo, nati, Cokanitu ku mahema a anthu awa oipa, musamakhudza kanthu kao kali konse, mungaonongeke m'zocimwa zao zonse.

27 Potero anakwera kucokera pozungulira mahema a Kora, Datani, ndi Abiramu, ndipo Datani ndi Abiramu anaturuka, naima pakhomo pa mahema ao, ndi akazi ao, ndi ana ao amuna, ndi makanda ao.

28 Ndipo Mose anati, Ndi ici mudzadziwa kuti Yehova wanditumiza ine kucita nchito izi zonse, ndi kuti sizifuma m'mtima mwanga mwanga.

29 Akafa anthu awa monga amafa anthu onse, kapena akasungika monga amasungika anthu onse, Yehova sananditumiza ine.

30 Koma Yehova akalenga cinthu catsopano, ndi nthaka ikayasama pakamwa pace, nikawameza ndi zonse ali nazo, nakatsikira iwo kumanda ali ndi moyo; pamenepo mudzadziwa kuti anthu awa anyoza Mulungu.

31 Ndipo kunali, pakutha iye kunena mau awa onse, nthaka inang'ambika pansi pao;

32 ndi dziko linayasama pakamwa pace ndi kuwameza, iwo ndi mabanja ao, ndi amuna ao onse akutsata Kora, ndi akatundu ao onse.

33 Comweco iwowa, ndi onse anali nao, anatsikira kumanda ali ndi moyo, ndi dziko linasunama pa iwo, ndipo anaonongeka pakati pa msonkhano.

34 Ndipo Aisrayeli onse akukhala pozinga pao anathawa pakumva kupfuula kwao; pakuti anati, Lingatimeze dziko ifenso.

35 Ndipo mota unaturuka kwa Yehova, ndi kunyeketsa amuna mazana awiri ndi makumi asanu aja akubwera naco cofukiza.

36 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

37 Nena ndi Eleazara mwana wa Aroni wansembe, kuti aphule mbale zofukiza pakati pa moto, nutaye makalawo uko kutali; pakuti ziri zopatulika;

38 mbale zofukizazo za iwo amene adacimwira moyo wao wao, ndipo azisule zaphanthiphanthi, zikhale cibvundikilo ca guwa la nsembe; popeza anabwera nazo pamaso pa Yehova, cifukwa cace zikhala zopatulika; ndipo zidzakhala cizindikilo kwa ana a Israyeli.

39 Ndipo Eleazara wansembe anatenga mbale zofukiza zamkuwa, zimene anthu opsererawo adabwera nazo; ndipo anazisula zaphanthiphanthi zikhale cibvundikilo ca guwala nsembe;

40 cikhale cikumbutso kwa ana a Israyeli, kuti mlendo, wosati wa mbeu ya Aroni, asasendere kucita cofukiza pamaso pa Yehova; angakhale monga Kora ndi khamu lace; monga Yehova adanena naye ndi dzanja la Mose.

41 Koma m'mawa mwace khamu lonse la ana a Israyeli anadandaula pa Mose ndi Aroni, nati, Mwapha anthu a Yehova, inu.

42 Ndipo kunali, posonkhanidwa khamulo kutsutsana nao Mose ndi Aroni, kuti anaceukira cihema cokomanako; taonani, mtambo unaciphimba, ndi ulemerero wa Yehova unaoneka.

43 Ndipo Mose ndi Aroni anadza kukhomo kwa cihema cokomanako.

44 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

45 Kwerani kucoka pakati pa khamu lino, kuti ndiwathe m'kamphindi. Pamenepo adagwa nkhope zao pansi.

46 Ndipo Mose anati kwa Aroni, Tenga mbale yako yofukiza, nuikemo mota wa ku guwa la nsembe, nuikepo cofukiza, nufulumire kumuka ku khamulo, nuwacitire cowatetezera; pakuti waturuka mkwiyo pamaso pa Yehova; wayamba mliri.

47 Ndipo Aroni anatenga monga Mose adanena, nathamanga kulowa pakati pa msonkhano; ndipo taonani, udayamba mliri pakati pa anthu; ndipo anaikapo cofukiza nawacitira anthu cowatetezera.

48 Ndipo anaima pakati pa akufa ndi amoyo; ndi mliri unaleka.

49 Koma akufa nao mliri ndiwo zikwi khumi ndi zinai mphambu mazana asanu ndi awiri, osawerenga aja adafera cija ca Kora.

50 Ndipo Aroni anabwera kwa Mose ku khomo la cihema cokomanako; ndi mliri unaleka.

17

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Nena ndi ana a Israyeli, nulandire kwa yense ndodo, banja liri onse la makolo ndodo imodzi, mafuko ao onse monga mwa mabanja a makolo ao azipereka ndodo, zikhale khumi ndi ziwiri; nulembe dzina la yense pa ndodo yace.

3 Ndipo ulembe dzina la Aroni pa ndodo ya Levi; pakuti pakhale ndodo imodzi pa mkuru yense wa nyumba za makolo ao.

4 Ndipo uziike m'cihema cokomanako, cakuno ca mboni, kumene ndikomana ndi inu.

5 Ndipo kudzali, kuti ndodo ya munthu ndimsankheyo, idzaphuka; ndipo ndidzadziletsera madandaulo a ana a Israyeli amene adandaula nao pa inu.

6 Ndipo Mose ananena ndi ana a Israyeli, ndipo akalonga ao onse anapereka, yense ndodo imodzi, monga mwa mabanja a makolo ao, ndodo khumi ndi ziwiri; ndi ndodo ya Aroni inakhala pakati pa ndodo zao.

7 Ndipo Mose anaika ndodozo pamaso pa Yehova m'cihema ca mboni.

8 Ndipo kunali m'mawa mwace, kuti Mose analowa m'cihema ca mboni; ndipo taonani, ndodo ya Aroni, ya pa banja la Levi, inaphuka, nionetsa timaani, nicita maluwa, nipatsa akatungurume.

9 Ndipo Mose anaturutsa ndodo zonse kuzicotsa pamaso pa Yehova, azione ana onse a Israyeli; ndipo anapenya, natenga yense ndodo yace.

10 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Bweza ndodo ya Aroni kulika cakuno ca mboni, isungike ikhale cizindikilo ca pa ana opikisana; kuti unelitsirizire madandaulo ao, kuti ungafe.

11 Ndipo Mose anacita monga Yehova adamuuza, momwemo anacita.

12 Pamenepo ana a Israyeli ananena ndi Mose, nati, Taonani, tikufa, tionongeka, tionongeka tonse.

13 Yense wakuyandikiza kacisi wa Yehova amwalira; kodi tidzatha nkufa?

18

1 Ndipo Yehova anati kwa Aroni, Iwe ndi ana ako amuna ndi banja la kholo lako pamodzi ndi iwe muzisenza mphulupulu ya malo opatulika; ndipo iwe ndi ana ako amuna pamodzi ndi iwe musenze mphulupulu ya nchito yanu ya nsembe.

2 Ndiponso abale ako, pfuko la Alevi, pfuko la kholo lako, uwayandikizitse pamodzi ndi iwe, kuti aphatikane ndi iwe, ndi kukutumikira; koma iwe ndi ana ako pamodzi ndi iwe mukhale ku khomo la cihema ca mboni.

3 Ndipo asunge udikiro wako, ndi udikiro wa cihema conse; koma asayandikize zipangizo za malo opatulika, ndi guwa la nsembe, kuti mungafe, iwo ndi inu.

4 Koma aziphatikana nawe, nazisunga udikiro wa cihema cokomanako, kucita nchito yonse ya cihema; koma mlendo asayandikize inu.

5 Ndipo musunge udikiro wa malo opatulika, ndi udikiro wa guwa la nsembe; kuti pasakhalenso mkwiyo pa ana a Israyeli.

6 Ndipo Ine, taonani, ndinatenga abale anu Alevi kuwacotsa pakati pa ana a Israyeli; ndiwo mphatso yanu, yopatsidwa kwa Yehova, kucita nchito ya cihema cokomanako.

7 Ndipo iwe ndi ana ako amuna pamodzi ndi iwe mucite nchito yanu ya nsembe, pa zonse za ku guwa la nsembe, ndi za m'kati mwa nsaru yocinga; ndipo mutumikire; ndikupatsani nchito yanu ya nsembe, utumiki wopatsika kwaulere; koma mlendo wakuyandikiza amuphe.

8 Ndipo Yehova ananena ndi Aroni, Ndipo taona, Ine ndakupatsa udikiro wa nsembe zanga zokweza, ndizo zopatulika zonse za ana a Israyeli; cifukwa ca kudzozedwaku ndazipereka kwa iwe, ndi kwa ana ako amuna, likhale lemba losatha.

9 Izi ndi zako pa zinthu zopatulikitsa, zosafika kumoto; zopereka: zao zonse, ndi nsembe zao zonse zaufa, ndi nsembe zao zonse zaucimo, ndi nsembe zao zonse zoparamula, zimene Andibwezera Ine, zikhale zopatulikitsa za iwe ndi za ana ako amuna.

10 Muzizidya izi monga zopatulikitsa; mwamuna yense adyeko; uziyese zopatulika.

11 Zako ndi izinso: nsembe yokweza ya mphatso yao, ndi nsembe zoweyula zonse za ana a Israyeli; ndazipereka kwa iwe, ndi kwa ana ako amuna ndi kwa ana ako akazi pamodzi ndi iwe, likhale lemba losatha; oyera onse a m'banja lako adyeko.

12 Mafuta onse okometsetsa, ndi vinyo watsopano, ndi tirigu yense wokometsetsa, zipatso zao zoyamba zimene aziperekako kwa Yehova, ndazipereka kwa iwe.

13 Zipatso zoyamba zonse ziri m'dziko mwao, zimene amadza nazo kwa Yehova, zikhale zako; oyera onse a m'banja lako adyeko.

14 Ziri zonse zoperekedwa ciperekere m'Israyeli ndi zako.

15 Ziri zonse zoyambira kubadwa mwa zamoyo zonse zimene abwera nazo kwa Yehova, mwa anthu ndi mwa nyama, ndi zako; koma munthu woyamba kubadwa uzimuombola ndithu; ndi nyama yodetsa yoyamba kubadwa uziiombola.

16 Ndipo zimene ziti zidzaomboledwa uziombole kuyambira za rowezi umodzi, monga mwa kuyesa kwako, pa ndarama za masekeli asanu, kuyesa sekeli wa malo opatulika, ndiwo magera makumi awiri.

17 Koma ng'ombe yoyamba kubadwa, kapena nkhosa yoyamba kubadwa, kapena mbuzi yoyamba kubadwa, usaziombola; ndizo zopatulika; uwace mwazi wace pa guwa la nserobe, ndi kufukiza mafuta ao, nsembe yamoto ya pfungo lokoma kwa Yehova.

18 Ndipo nyama yace ndi yako, ndiyo nganga ya nsembe yoweyula ndi mwendo wathako wa kulamanja, ndizo zako.

19 Nsembe zokweza zonse za zinthu zopatulika, zimene ana a Israyeli azikweza kwa Yehova, ndazipereka kwa iwe, ndi kwa ana ako amuna ndi kwa ana ako akazi pamodzi ndi iwe, likhale lemba losatha; ndilo pangano lamcere losatha, pamaso pa Yehova, kwa iwe ndi mbeu zako pamodzi ndi iwe.

20 Ndipo Yehova ananena ndi Aroni, Ulibe colowa m'dziko lao, ulibe gawo pakati pao; Ine ndine gawo lako ndi colowa cako pakati pa ana a Israyeli.

21 Ndipo taonani, ndawaninkha ana a Levi limodzi la magawo khumi mwa zonse m'Israyeli, likhale colowa cao, mphotho ya pa nchito yao alikuicita, nchito ya cihema cokomanako.

22 Ndipo kuyambira tsopano ana a Israyeli asayandikize cihema cokomanako, angamasenze ucimo kuti angafe.

23 Koma Alevi azicita nchito ya cihema cokomanako, iwo ndiwo azisenza mphulupulu yao; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu; ndipo asakhale naco colowa pakati pa ana a Israyeli.

24 Popeza ndapatsa Alevi limodzi la magawo khumi, la ana a Israyeli, limene apereka nsembe, yokweza kwa Yehova, likhale colowa cao; cifukwa cace ndanena nao, Asadzakhale naco colowa mwa ana a Israyeli.

25 Ndipo Yehova ananena ndil Mose, nati,

26 Unenenso ndi Alevi, nuti nao, Pamene mulandira kwa ana a Israyeli, limodzi la magawo khumi limene ndakupatsani likhale colowa canu cocokera kwao, muziperekako nsembe yokweza ya Yehova, limodzi la magawo khumi la limodzi la magawo khumi.

27 Ndipo akuyesereninso nsembe yanu yokweza monga tirigu wa padwale, monga mopondera mphesa modzala.

28 Momweno inunso muzipereka kwa Yehova nsembe yokweza yocokera ku magawo anu onse a magawo khumi, a zonse muzilandira kwa ana a Israyeli; ndipo muperekeko nsembe yokweza ya Yehova kwa Aroni wansembe.

29 Mupereke nsembe zokweza zonse za Yehova kuzitenga ku mphatso zanu zonse, kusankhako zokometsetsa ndizo zopatulika zace.

30 Cifukwa cace unene nao, Pamene mukwezako zokometsetsa zace, zidzayesedwanso kwa Alevi ngati zipatso za padwale, ndi zipatso za mopondera mphesa,

31 Ndipo muzidye pamalo ponse, inu ndi a pabanja panu; popeza ndizo mphotho yanu mwa nchito yanu m'cihema cokomanako.

32 Ndipo simudzasenzapo ucimo, mutakwezako zokometsetsa zace; ndipo musamaipsa zinthu zopatulika za ana a Israyeli, kuti mungafe.

19

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,

2 Ili ndi lemba la cilamulo Yehova adalamuliraci, ndi kuti, Nena ndi ana a Israyeli kuti azikutengera ng'ombe ramsoti yofiira, yangwiro yopanda enema, yosamanga m'goli;

3 ndipo muipereke kwa Eleazara wansembe, naiturutse iye kunja kwa cigono, ndipo wina aiphe pamaso pace.

4 Ndipo Eleazara wansembe atengeko mwazi wace ndi cala cace, nawazeko mwazi wace kasanu ndi kawiri pakhomo pa cihema cokomanako.

5 Pamenepo atenthe ng'ombe yamsotiyo pamaso pace; atenthe cikopa cace ndi nyama yace, ndi mwazi wace, pamodzi ndi cipwidza cace.

6 Ndipo wansembe atenge mtengo wamkungudza, ndi hisope, ndi ubweya wofiira, naziponye pakati pa mota irikupsererapo ng'ombe yamsoti.

7 Pamenepo wansembe atsuke zobvala zace, nasambe thupi lace ndi madzi; ndipo atatero alowenso kucigono; koma wansembeyo adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.

8 Ndipo iye wakutentha ng'ombeyo atsuke zobvala zace, nasambe thupi lace ndi madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.

9 Ndipo munthu woyera aole mapulusa a ng'ombe ya msotiyo, nawaike kunja kwa cigono, m'malo moyera: ndipo awasungire khamu la ana a lsrayeli akhale a madzi akusiyanitsa; ndiwo nsembe yaucimo.

10 Ndipo wakuola mapulusayo a ng'ombe ya msoti atsuke zobvala zace, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo; ndipo likhale lemba losatha kwa ana a Israyeli, ndi kwa mlendo wakukhala pakati pao.

11 Iye wakukhudza mtembo wa munthu ali yense adzakhala wodetsedwa masiku asanu ndi awiri;

12 iyeyo adziyeretse nao tsiku lacitatu, ndi pa tsiku lacisanu ndi ciwiri adzakhala woyera; koma akapanda kudziyeretsa tsiku lacitatu, sadzakhala woyera tsiku lacisanu ndi ciwiri.

13 Ali yense wakukhudza mtembo wa munthu ali yense wakufa, osadziyeretsa, aipsa kacisi wa Yehova; amsadze munthuyo kwa Israyeli; popeza sanamwaza madzi akusiyanitsa; ndiye wodetsedwa; kudetsedwa kwace kukali pa iye.

14 Cilamulo ndi ici: Munthu akafa m'hema, yense wakulowa m'hemamo, ndi yense wakukhala m'hemamo, adzakhala wodetsedwa masiku asanu ndi awiri.

15 Ndi zotengera zonse zobvundukuka, zopanda cibvundikilo comangikapo, ziri zodetsedwa.

16 Ndipo ali yense wakukhudza munthu wophedwa ndi lupanga, kapena mtembo, kapena pfupa la munthu, kapena manda, pathengo poyera, adzakhala wodetsedwa masiku asanu ndi awiri.

17 Ndipo atengereko wodetsedwayo mapulusa akupsererawo a nsembe yaucimo, nathirepo m'cotengera madzi oyenda;

18 ndi munthu woyera atenge hisope, nambviike m'madzimo, ndi kuwawaza pahema ndi pa zotengera zonse, ndi pa anthu anali pomwepo, ndi pa iye wakukhudza pfupa, kapena wophedwa, kapena wakufa, kapena Manda.

19 Ndipo woyerayo awaze pa wodetsedwayo tsiku lacitatu, ndi tsiku lacisanu ndi ciwiri; ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri amyeretse; ndipo atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala woyera madzulo.

20 Koma munthu wakukhala wodetsedwa, koma wosadziyeretsa, azimsadza munthuyo pakati pa msonkhano, popeza waipsa malo opatulika a Yehova; sanamwaza madzi akusiyanitsa; ndiye wodetsedwa.

21 Ndipo likhale kwa iwo lemba losatha; kuti iye wakuwaza madzi akusiyanitsa azitsuka zobvala zace; ndi iye wakukhudza madzi akusiyanitsa adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.

22 Ndipo ciri conse munthu wodetsedwa acikhudza cidzakhala codetsedwa; ndi munthu wakucikhudza adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.

20

1 Ndipo ana a Israyeli, ndilo khamu lonse, analowa m'cipululu ca Zini mwezi woyamba; ndipo anthu anakhala m'Kadesi; kumeneko anafa Miriamu, naikidwakomweko.

2 Ndipo khamulo linasowa madzi; pamenepo anasonkhana kutsutsana nao Mose ndi Aroni.

3 Ndipo anthu anatsutsana ndi Mose, nanena, nati, Mwenzi titangomwalira muja abale athu anamwalira pamaso pa Yehova!

4 Mwalowa nao bwanji msonkhano wa Yehova m'cipululu muno, kuti tifere mommuno, ife ndi zoweta zathu?

5 Ndipo munatikwezeranji kutiturutsa m'Aigupto, kutilowetsa m'malo oipa ano? Si malo a mbeu awa, kapena mkuyu, kapena mpesa kapena makangaza; ngakhale madzi akumwa palibe.

6 Ndipo Mose ndi Aroni anacoka pamaso pa msonkhano kumka ku khomo la cihema cokomanako, nagwa nkhope zao pansi; ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera iwo.

7 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

8 Tenga ndodoyo, nusonkhanitse khamulo; iwe ndi Aroni mbale wako, munene ndi thanthwe pamaso pao, kuti liwapatse madzi; potero uwaturutsire madzi m'thanthwe, ndi kumwetsa khamu la anthu ndi zoweta zao.

9 Ndipo Mose anatenga ndodoyo kuicotsa pamaso pa Yehova, monga iye anamuuza iye.

10 Ndipo Mose ndi Aroni anasonkhanitsa msonkhano pathanthwe, nanena nao iye, Tamvanitu, opikisana naye inu; kodi tikuturutsireni madzi m'thanthwe umu?

11 Ndipo Mose anasamula dzanja lace, napanda thanthwe kawiri ndi ndodo; ndipo madzi anaturukamo ocuruka, ndi khamulo linamwa, ndi zoweta zao zomwe.

12 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, Popeza simunandikhulupirira Ine, kundipatula Ine pamaso pa ana a Israyeli, cifukwa cace simudzalowetsa msonkhano uwu m'dziko ndinawapatsali.

13 Awa ndi madzi a Meriba; popeza ana a Israyeli anatsutsana ndi Yehova, ndipo anapatulidwa mwa iwowa.

14 Pamenepo Mose anatumiza amithenga ocokera ku Kadesi kumuka kwa mfumu ya Edomu, ndi kuti, Atero mbale wanu Israyeli, Mudziwa zowawa zonse zinatigwera;

15 kuti makolo athu anatsikira kumka ku Aigupto, ndipo tinakhala m'Aigupto masiku ambiri; ndipo Aaigupto anacitira zoipa ife, ndi makolo athu.

16 Pamenepo tinapfuulira kwa Yehova, ndipo anamva mau athu, natuma mthenga, natiturutsa m'Aigupto; ndipo, taonani, tiri m'Kadesi, ndiwo mudzi wa malekezero a malire anu.

17 Tipitetu pakati pa dziko lanu; sitidzapitira pamunda, kapena munda wampesa, sitidzamwa madzi a m'zitsime; tidzatsata mseu wacifumu; sitidzapatukira kulamanja kapena kulamanzere, mpaka titapitirira malire anu.

18 Koma Edomu ananena naye, Usapitire pakati pa ine, kuti ndingaturuke kukomana nawe ndi lupanga.

19 Ndipo ana a Israyeli ananena naye, Tidzatsata mseu; ndipo tikakamwa madzi ako, ine ndi zoweta zanga, pamenepo ndidzapatsa mtengo wace; sindifuna kanthu kena koma kungopitapo mwa njira.

20 Koma anati, Usapitirepo. Ndipo Edomu anaturukira kukumana naye ndi anthu ambiri, ndi dzanja lamphamvu.

21 Potero Edomu anakana kulola Israyeli kupitira pa malire ace; cifukwa cace Aisrayeli anampatukira.

22 Ndipo anayenda ulendo kucokera ku Kadesi; ndi ana a Israyeli, ndilo khamu lonse, anadza ku phiri la Hori.

23 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni m'phiri la Hori, pa malire a dziko la Edomu, ndi kuti,

24 Aroni adzaitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wace; pakuti sadzalowa m'dziko limene ndapatsa ana a Israyeli, popeza munapikisana ndi mau anga ku madzi a Meriba.

25 Tenga Aroni ndi Eleazara mwana wace, nukwere nao m'phiri la Hori;

26 nubvule Aroni zobvala zace, numbveke Eleazara mwana wace; ndipo Aroni adzaitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wace, nadzafa komweko.

27 Pamenepo Mose anacita monga adamuuza; ndipo anakwera m'phiri la Hori pamaso pa khamu lonse.

28 Ndipo Mose anabvula Aroni zobvala zace, nabveka Eleazara mwana wace; ndipo Aroni anafa pomwepo pamwamba pa phiri, Pamenepo Mose ndi Eleazara anatsika m'phirimo.

29 Pamene khamu lonse linaona kuti Aroni adamwalira, anamlira Aroni masiku makumi atatu, ndiyo mbumba yonse ya Israyeli.

21

1 Pamene Mkanani, mfumu ya Aradi, wokhala kumwela, anamva kuti Israyeli anadzera njira ya azondi, anathira nkhondo pa Israyeli, nagwira ena akhale ansinga.

2 Ndipo Israyeli analonjeza cowinda kwa Yehova, nati, Mukadzaperekatu anthu awa m'dzanja langa, ndidzaononga midzi yao konse.

3 Ndipo Yehova anamvera mau a Israyeli, napereka Akanani; ndipo anawaononga konse ndi midzi yao yomwe; nacha dzina lace la malowo Horima.

4 Ndipo anayenda ulendo kucokera ku phiri la Hori, nadzera njira ya Nyanja Yofiira, kupaza ku dziko la Edomu; ndi mtima wa anthu unada cifukwa ca njirayo.

5 Ndipo anthu ananena motsutsana ndi Mulungu, ndi Mose, ndi kuti, Mwatikwezeranji kuticotsa ku Aigupto kuti tifere m'cipululu? pakuti mkate ndi madzi palibe, ndi mtima wathu walema nao mkate wacabe uwu.

6 Pamenepo Yehova anatumiza njoka zamoto pakati pa anthu, ndipo zinaluma anthu; nafapo anthu ambiri a Israyeli.

7 Ndipo anthu anadza kwa Mose, nati, Tacimwa, popeza tinanena motsutsana ndi Yehova, ndi inu; pempherani kwa Yehova kuti aticotsere njokazi. Ndipo Mose anawapempherera anthu.

8 Pamenepo Yehova anati kwa Mose, Upange njoka yamoto; nulike pa mtengowace; ndipo kudzali, kuti onse olumwa, akuipenya njokayo, adzakhala ndi moyo.

9 Ndipo Mose anapanga njoka yamkuwa, naiika pamtengo; ndipo kunali, njoka itamluma munthu ali yense, nakapenyetsetsa iye pa njoka yamkuwa, nakhala ndi moyo.

10 Pamenepo ana a Israyeli anayenda ulendo, namanga mahema m'Oboti.

11 Ndipo anacoka ku Oboti, namanga mahema ku Iyebarimu, m'cipululu cakuno ca Moabu, koturukira dzuwa.

12 Pocokapo anayenda ulendo, namanga mahema m'cigwa ca Zaredi.

13 Atacokako anayenda ulendo, namanga mahema tsidya tina la Arinoni, wokhala m'cipululu, wogwera ku malire a Aamori; popeza Arinoni ndiwo malire a Moabu, pakati pa Moabu ndi Aamori.

14 Cifukwa cace, ananena m'buku la Nkhondo za Yehova, Vahebi m'Sufa, Ndi miyendo ya Arinoni;

15 Ndi zigwa za miyendoyo Zakutsikira kwao kwa Ari, Ndi kuyandikizana ndi malire a Moabu.

16 Ndipo atacokapo anamuka ku Been, ndico citsime cimene Yehova anacinena kwa Mose, Sonkhanitsa anthu, ndipo ndidzawapatsa madzi.

17 Pamenepo Israyeli anayimba nyimbo iyi: Tumphuka citsime iwe; mucithirire mang'ombe;

18 Citsime adakumba mafumu, Adacikonza omveka a anthu; Atanena mlamuli, ndi ndodo zao. Ndipo atacoka kucipululu anamuka ku Matana;

19 atacoka ku Matana ku Nahaliyeli; atacoka ku Nahaliyeli ku Bamoti;

20 atacoka ku Bamoti ku cigwa ciri m'dziko la Moabu, ku mutu wa Pisiga, popenyana ndicipululu.

21 Ndipo Israyeli anatuma amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, ndi kuti,

22 Ndipitire pakati pa dziko lako; sitidzapatuka kulowa m'munda, kapena m'munda wampesa, sitidzamwako madzi a m'zitsime; tidzatsata mseu wacifumu, kufikira tapitirira malire ako.

23 Ndipo Sihoni sanalola Israyeli apitire m'malire ace; koma Sihoni anamemeza anthu ace onse, nadzakomana naye Israyeli m'cipululu, nafika ku Jahazi, nathira nkhondo pa Israyeli.

24 Ndipo Israyeli anamkantha ndi lupanga lakuthwa, nalanda dziko lace likhale lao lao, kuyambira Arinoni kufikira Yaboki, kufikira ana ai Amoni; popeza malire a ana a Amoni ndiwo olimba.

25 Ndipo Israyeli analanda midzi iyi yonse; nakhala Israyeli m'midzi yonse ya Aamori; m'Hesiboni ndi miraga yace yonse.

26 Popeza Hesiboni ndiwo mudzi wa Sihoni mfumu ya Aamori, imene idathira nkhondo pa mfumu idafayo ya Moabu, nilanda dziko lace m'dzanja lace kufikira Arinoni.

27 Cifukwa cace iwo akunena mophiphiritsa akuti, Idzani ku Hesiboni, Mudzi wa Sihoni umangike, nukhazikike:

28 Popeza moto unaturuka m'Hesiboni, Cirangali ca mota m'mudzi wa Sihoni; Catha Ari wa Moabu, Eni misanje ya Arinoni.

29 Tsoka kwa iwe, Moabu! Mwaonongeka, anthu a Kemosi inu, Anapereka ana ace amuna opulumuka, Ndi ana ace akazi akhale ansinga, Kwa Sihoni mfumu ya Aamori.

30 Tinawagwetsa; Hesiboni waonongeka kufikira ku Diboni, Ndipo tinawapululutsa kufikira ku Nofa, Ndiwo wakufikira ku Medeba.

31 Comweco Israyeli anakhala m'dziko la Aamori.

32 Ndipo Mose anatumiza anthu akazonde Yazere, nalanda miraga yace, napitikitsa Aamori a komweko.

33 Ndipo anatembenuka nakwera kudzera njira ya ku Basanu; ndipo Ogi mfumu ya ku Basana anaturuka kukumana nao, iye ndi anthu ace onse, kudzacita nao nkhondo ku Edreyi.

34 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Usamuopa; popeza ndampereka m'manja mwako, iye ndi anthu ace onse, ndi dziko lace; umcitire monga umo unacitira Sihoni mfumu ya Aamori anakhalayo ku Hesiboni.

35 Ndipo anamkantha iye, ndi ana ace amuna ndi anthu ace onse, kufikira sanatsala ndi mmodzi yense; nalanda dziko lace likhale lao lao.

22

1 Ndipo ana a Israyeli anayenda ulendo, namanga mahema m'zigwa za Moabu, tsidya la Yordano ku Yeriko.

2 Ndipo Balaki mwana wa Zipori anaona zonse Israyeli anacitira Aamori.

3 Ndipo Moabu anacita mantha akuru ndi anthuwo, popeza anacuruka; nada mtima Moabu cifukwa ca ana a Israyeli.

4 Ndipo Moabu anati kwa akuru a Midyani, Tsopano msonkhano uwu udzanyambita zonse ziri pozinga pathu, monga ng'ombe zinyambita msipu wa kubusa. Ndipo Balaki mwana wa Zipori anali mfumu ya Moabu masiku amenewo.

5 Ndipo anatuma amithenga kwa Balamu mwana wa Beori, ku Petori, wokhala kumtsinje, wa dziko la anthu a mtundu wace, kuti amuitane, ndi kuti, Taonani, anaturuka anthu m'dziko la Aigupto; taonani, aphimba nkhope ya dziko, nakhala popenyana ndi ine.

6 Ndipo tsopano, idzatu, nunditembererere anthu awa; popeza andiposa mphamvu; kapena ndidzawalaka, kuti tiwakanthe, ndi kuti ndiwapitikitse m'dziko; pakuti ndidziwa kuti iye amene umdalitsa adalitsika, ndi iye amene umtemberera atemberereka.

7 Ndipo akuru a Moabu ndi akuru a Midyani anamuka ndi mphotho za maula m'dzanja lao; anadza kwa Balamu, nanena naye mau a Balaki.

8 Ndipo ananena nao, Mugone kuno usiku uno, ndidzakubwezerani mau, monga Yehova adzanena ndi ine; pamenepo mafumu a Moabu anagona ndi Balamu.

9 Ndipo Mulungu anadza kwa Balamu, nati, Anthu awa ali ndi iwe ndiwo ayani?

10 Ndipo Balamu anati kwa Mulungu, Balaki mwana wa Zipori mfumu ya Moabu, anatumiza kwa ine, ndi kuti,

11 Taonani, anthu awa adaturuka m'Aigupto aphimba nkhope ya dziko, idzatu unditembererere awa; kapena ndidzakhoza kulimbana nao nkhondo, ndi kuwapitikitsa.

12 Koma Mulungu anati kwa Balamu, Usapita nao; usatemberera anthuwa; pakuti adalitsika.

13 Ndipo Balamu anauka m'mawa, nati kwa akalonga a Balaki, Mukani ku dziko lanu; popeza Yehova andikaniza kuti ndisapite nanu,

14 Pamenepo akalonga a Moabu ananyamuka, nafika kwa Balaki, nati, Alikukana Balamu kudza nafe.

15 Koma Balaki anaonjeza kutumanso akalonga, ocuruka, ndi omveka koposa awa.

16 Ndipo anadza kwa Balamu, nati kwa iye, Atero Balaki mwana wa Zipori, Pasakhaletu cinthu cakukuletsa kudza kwa ine;

17 popeza ndidzakucitira ulemu waukuru, ndipo zonse unena ndi ine ndidzacita; cifukwa cace idzatu, unditembererere anthu awa.

18 Ndipo Balamu, anayankha nati kwa anyamata a Balaki, Cinkana Balaki andipatsa nyumba yace yodzala ndi siliva ndi golidi, sindikhoza kutumpha mau a Yehova Mulungu wanga, kucepsako kapena kuonjezako.

19 Ndikupemphani, tsono, khalani pano inu usiku uno womwe; kuti ndidziwe comwe Yehova adzanenanso nane.

20 Ndipo Mulungu anadza kwa Balamu usiku, nanena naye, Akadza kukuitana anthuwa, nyamuka, kumka nao, koma mau okha okha ndinena ndi iwe, ndiwo ukacite.

21 Pamenepo Balamu anauka m'mawa namanga buru wace, namuka nao akalonga a ku Moabu.

22 Koma anapsa mtima Mulungu cifukwa ca kupita iye, ndipo mthenga wa Yehova anadziika m'njira wotsutsana naye, Ndipo anali wokwera pa buru wace, ndi anyamata ace awiri anali naye,

23 Ndipo buruyo anaona mthenga wa Yehova alikuima m'njira, ndi lupanga lace ku dzanja lace; ndi buru anapatuka m'njira, nalowa kuthengo; ndipo Balamu anampanda buru kumbwezera kunjira.

24 Pamenepo mthenga wa Yehova anaima m'njira yopapatiza ya minda yampesa; mbali yina kuli linga, mbali yina linga.

25 Ndipo buru anaona mthenga wa Yehova, nadzikankhira kulinga, nakanikiza phazi la Balamu kulinga; ndipo anampandanso.

26 Pamenepo mthenga wa Yehova anapitiriranso, naima popapatiza, popanda popatukira kulamanja kapena kulamanzere.

27 Ndipo buru wace anaona mthenga wa Yehova, nagona pansi, Balamu ali pamsana pace; ndipo Balamu adapsa mtima, nampanda buru ndi ndodo.

28 Ndipo Yehova anatsegula pakamwa pace pa buru, nati uyu kwa Balamu, Ndakucitanji, kuti wandipanda katatu tsopano?

29 Pamenepo Balamu anati kwa buru, Cifukwa wandipeputsa; mukadakhala lupanga m'dzanja langa tsopano, ndikadakupha iwe.

30 Ndipo buru anati kwa Balamu, Si ndine buru wako amene umayenda wokwera pa ine ciyambire ndiri wako kufikira lero lino? Kodi ndikakucitira cotere ndi kale lonse? Ndipo anati, Iai.

31 Pamenepo Yehova anapenyetsa maso a Balamu, naona iye mthenga wa Yehova alikuima m'njira, lupanga losolola liri kudzanja, ndipo anawerama mutu wace, nagwa nkhope yace pansi.

32 Ndipo mthenga wa Yehova ananena naye, Wapandiranji buru wako katatu tsopano? taona, ndaturuka kuti nditsutsane nawe popeza njira iyi ikugwetsa camtu pamaso panga;

33 koma buru anandiona, nandipatukira nthawi izi zitatu pondiona; akadapanda kundipatukira, ndikadakupha iwe ndithu, ndi kumsunga iye wamoyo.

34 Pamenepo Balamu anati kwa mthenga wa Yehova, Ndacimwa, popeza sindinadziwa kuti munaima mondiletsa m'njira; ndipo tsopano, ngati cikuipirani, ndibwerera.

35 Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa Balamu, Pita nao anthuwa; koma mau okha okha ndinena ndi iwe, ndiwo ukanene, Potero Balamu anamuka nao akalonga a Balaki.

36 Pamene Balaki anamva kuti wafika Balamu, anamturukira kukakomana naye ku mudzi wa Moabu, wokhala m'mphepete mwa Arinoni, ndiwo ku malekezero a malire ace.

37 Ndipo Balaki anati kwa Balamu, Kodi sindinatumiza kwa iwe ndithu kukakuitana? Unalekeranji kudza kwa ine? sindikhoza kodi kukucitira ulemu?

38 Ndipo Balamu anati kwa Balaki, Taonani, ndafika kwa inu; ngati ndiri nayo mphamvu konse tsopano kunena kanthu? mau amene Mulungu aike m'kamwa mwanga ndiwo ndidzanena.

39 Ndipo Balamu anamuka ndi Balaki, nafika iwo ku Kiriyati Huzoti.

40 Pamenepo Balaki anapha ng'ombe ndi nkhosa, natumizira Balamu, ndi akalonga okhala naye.

41 Ndipo kunali kuti m'mawa, Balaki anatenga Balamu, nakwera nave ku misanje ya Baala, ndi kumeneko anaona malekezero a anthuwo.

23

1 Ndipo Balamu anati kwa Balaki, Ndimangireni kuno maguwa a nsembe asanu ndi awiri, nimundikonzere kuno ng'ombe zisanu ndi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri.

2 Ndipo Balaki anacita monga Balamu ananena; ndipo Balaki ndi Balamu anapereka pa guwa la nsembe liri lonse ng'ombe ndi nkhosa yamphongo.

3 Ndipo Balamu anati kwa Balaki, Imani pa nsembe yopsereza yanu, ndipite ine, kapena Yehova akadza kukomana ndi ine; ndipo cimene akandionetsa ine ndidzakufotokozerani. Ndipo anapita pamsanje poyera,

4 Pamenepo Mulungu anakomana ndi Balamu; ndipo ananena ndi iye, Ndakonza maguwa a nsembe asanu ndi awiri, ndipo ndapereka ng'ombe ndi nkhosa yamphongo pa guwa la nsembe liri lonse.

5 Ndipo Yehova anaika mau m'kamwa mwa Balamu, nati, Bwerera kwa Balaki, nukanene cakuti cakuti.

6 Ndipo anabwerera kwa iye, ndipo, taonani, analikuima pa nsembe yopsereza yace, iye ndi akalonga onse a Moabu.

7 Ndipo ananena fanizo lace, nati, Ku Aramu ananditenga Balaki, Mfumu ya Moabu ananditenga ku mapiri a kum'mawa; Idza, udzanditembererere Yakobo. Idza, nudzanyoze Israyeli.

8 Ndidzatemberera bwanji amene Mulungu sanamtemberera? Ndidzanyoza bwanji, amene Yehova sanamnyoza?

9 Pakuti, pokhala pamwamba pa matanthwe ndimpenya, Pokhala pa zitunda ndimuyang'ana; Taonani, ndiwo anthu akukhala paokha. Osadziwerengera pakati pa amitundu ena,

10 Adzawerenga ndani pfumbi la Yakobo, Kapena kuwerenga limodzi la magawo anai la Israyeli? Ndipo ine ndife monga amafa aongoka mtima, Citsiriziro canga cifanane naco cace!

11 Pamenepo Balaki anati kwa Balamu, Wandicitiranji? Ndinakutenga utemberere adani anga, ndipo taona, wawadalitsa ndithu.

12 Ndipo anayankha nati, Cimene aciika m'kamwa mwanga Yehova, sindiyenera kodi kunena ici?

13 Ndipo Balaki anati naye, Tiyetu, upite nane kumalo kwina, kumene ukawaona; udzaona malekezero ao okha, osawaona onse; ndipo pokhala pamenepo ukanditembererere iwo.

14 Ndipo anamuka naye ku thengo la Zofimu, pamwamba pa Pisiga, namangako maguwa a nsembe asanu ndi awiri, napereka ng'ombe ndi nkhosa pa guwa la nsembe liri lonse.

15 Ndipo anati kwa Balaki, Imani pano pa nsembe yopsereza yanu, ndipite ine ndikakomane ndi iye uko.

16 Ndipo Yehova anakomana naye Balamu, naika mau m'kamwa mwace, nati, Bwerera kwa Balaki, nukanene cakuti cakuti.

17 Ndipo anadza kuli iye, ndipo taona, analikuima pa nsembe yace yopsereza, ndi akalonga a Moabu pamodzi naye. Ndipo Balaki anati kwa iye, Wanenanji Yehova?

18 Ndipo ananena fanizo lace, nati, Ukani, Balaki, imvani; Ndimvereni, mwana wa Zipori;

19 Mulungu sindiye munthu, kuti aname; Kapena mwana wa munthu, kuti aleke; Kodi anena, osacita?

20 Kapena kulankhula, osacitsimikiza? Taonani, ndalandira mau akudalitsa, Popeza iye wadalitsa, sinditha kusintha.

21 Sayang'anira mphulupulu iri m'Yakobo, Kapena sapenya kupulukira kuli m'lsrayeli. Yehova Mulungu wace ali ndi iye, Ndi mpfuu wa mfumu uli pakati pao,

22 Mulungu awaturutsa m'Aigupto; Mphamvu yace ikunga ya njati.

23 Pakuti palibe nyanga pakati pa Yakobo, Kapena ula mwa Israyeli; Pa nyengo yace adzanena kwa Yakobo ndi Israyeli, Cimene Mulungu acita.

24 Taonani, anthuwo auka ngati mkango waukazi, Nadzitukumula ngati mkango waumuna: Sugonansokufikira utadya nyama yogwira, Utamwa mwazi wa zophedwa.

25 Ndipo Balaki anati kwa Balamu, Usawatemberera konse, kapena kuwadalitsa konse.

26 Koma Balamu anayankha nati kwa Balaki, Sindinakuuzani ndi kuti, Ciri conse acinena Yehova, comweco ndizicita?

27 Ndipo Balaki anati kwa Balamu, Tiyetu, ndimuke nawe kumalo kwina; kapena kudzakomera pamaso pa Mulungu kuti unditembererere iwo pokhala kumeneko.

28 Ndipo Balaki anamka naye Balamu pamwamba pa Peori, popenyana ndi cipululu.

29 Ndipo Balamu anati kwa Balaki, Mundimangire pano maguwa a nsembe asanu ndi awiri, nimundikonzere pano ng'ombe zisanu ndi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri.

30 Ndipo Balaki anacita monga adanena Balamu, napereka ng'ombe ndi nkhosa yamphongo pa guwa la nsembe liri laose.

24

1 Pamene Balamu anaona kuti kudakomera pamaso pa Yehova kudalitsa Israyeli, sanamuka, monga nthawi zija zina, ku nyanga zolodzera, koma anayang'ana nkhope yace kucipululu.

2 Ndipo Balamu anakweza maso ace, naona Israyeli alikukhala monga mwa mafuko ao; ndipo mzimu wa Mulungu unadza pa iye.

3 Pamenepo ananena fanizo lace, nati, Balamu mwana wa Beori anenetsa, Ndi munthuyo anatsinzina maso anenetsa;

4 Wakumva mau a Mulungu anenetsa, Wakuona masomphenya a Wamphamvuyonse, Wakugwa pansi maso ace openyuka:

5 Ha! mahema ako ngokoma, Yakobo; Zokhalamo zako, Israyeli!

6 Ziyalika monga zigwa, Monga minda m'mphepete mwanyanja, Monga khonje waoka Yehova, Monga mikungudza m'mphepete mwa madzi.

7 Madzi adzayenda naturuka m'zotungira zace, Ndi mbeu zace zidzakhala ku madzi ambiri, Ndi mfumu yace idzamveka koposa Agagi, Ndi ufumu wace udzamveketsa.

8 Mulungu amturutsa m'Aigupto; Ali nayo mphamvu yonga ya njati; Adzawadya amitundu, ndiwo adani ace. Nadzaphwanya mafupa ao, Ndi kuwapyoza ndi mibvi yace.

9 Anaunthama, nagona pansi ngati mkango, Ngati mkango waukazi; adzamuutsa ndani? Wodalitsika ali yense wakudalitsa iwe, Wotemberereka ali yense wakutemberera iwe.

10 Pamenepo Balaki anapsa mtima pa Balamu, naomba m'manja; ndipo Balaki anati kwa Balamu, Ndinakuitana kutemberera adani ansa, ndipo unawadalitsa ndithu katatu tsopano.

11 Cifukwa cace thawira ku malo ako tsopano; ndikadakucitira ulemu waukuru; koma, taona, Yehova wakuletsera ulemu.

12 Ndipo Balamu anati kwa Balaki, Kodi sindinauzanso amithenga anu amene munawatumiza kwa ine, ndi kuti,

13 Cinkana Balaki akandipatsa nyumba yace yodzala ndi siliva ndi golidi, sindikhoza kutumpha mau a Yehova, kucita cokoma kapena coipa ine mwini wace; conena Yehova ndico ndidzanena ine?

14 Ndipo tsopano, taonani, ndimuka kwa anthu a mtundu wanga; tiyeni, ndidzakulangizani, ndi kukuuzani zimene anthu awa adzacitira anthu anu, masiku otsiriza.

15 Ndipo ananena fanizo lace, nati, Balamu mwana wa Beori anenetsa, Ndi munthu wotsinzina masoyo anenetsa;

16 Anenetsa wakumva mau a Mulungu, Ndi kudziwa nzeru ya Wam'mwambamwamba, Wakuona masomphenya a Wamphamvuyonse, Wakugwa pansi wopenyuka maso;

17 Ndimuona, koma tsopano ai; Ndimpenya, koma si pafupi ai; Idzaturuka nyenyezi m'Yakobo, Ndi ndodo yacifumu idzauka m'Israyeli, Nidzakantha malire a Moabu, Nidzapasula ana onse a Seti,

18 Ndi Edomu adzakhala ace ace, Seiri lomwe lidzakhala lace lace, ndiwo adani ace;

19 Koma Israyeli adzacita zamphamvu. Ndipo wina woturuka m'Yakobo adzacita ufumu; Nadzapasula otsalira m'mudzi.

20 Ndipo anayang'ana ku Amaleki, nanena fanizo lace, nati, Amaleki ndiye woyamba wa amitundu; Koma citsiriziro cace, adzaonongeka ku nthawi zonse.

21 Ndipo anayang'ana Akeni, nanena fanizo lace, nati, Kwanu nkokhazikika, Wamanga cisa cako m'thanthwe.

22 Koma Kaini adzaonongeka, Kufikira Asuri adzakumanga nsinga.

23 Ndipo ananena fanizo lace, nati, Ha! adzakhala ndi moyo ndani pakucita ici Mulungu?

24 Koma zombo zidzafika kucokera ku doko la Kitimu, Ndipo adzasautsa Asuri, nadzasautsa Ebere, Koma iyenso adzaonongeka.

25 Ndipo Balamu anauka, namuka nabwerera kumalo kwace; ndi Balaki yemwe anamka njira yace.

25

1 Ndipo Israyeli anakhala m'Sitimu, ndipo anthu anayamba kucita cigololo ndi ana akazi a Moabu;

2 popeza anaitana anthuwo adze ku nsembe za milungu yao; ndipo anthuwo anadya, nagwadira milungu yao.

3 Pamene Israyeli anaphatikana ndi Baala Peori, Mulungu anapsa mtima pa Israyeli.

4 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Gwira akuru onse a anthu nuwapacikire Yehova, pali dzuwa poyera, kuti mkwiyo waukali wa Yehova ucoke kwa Israyeli.

5 Ndipo Mose anati kwa oweruza a Israyeli, Iphani, yense anthu ace adapatikanawo ndi Baala-Peori.

6 Ndipo, taonani, anadza wina wa ana a Israyeli, nabwera naye mkazi Mmidyani kudza naye kwa abale ace, pamaso pa Mose, ndi pamaso pa khamu lonse la ana a Israyeli, pakulira iwo pa khomo la cihema cokomanako.

7 Pamene Pinehasi mwana wa Eleazara, mwana wa Aroni wansembe, anaciona, anauka pakati pa khamu, natenga nthungo m'dzanja lace;

8 natsata munthu M-israyeli m'hema, nawamoza onse awiri, munthu M-israyeli ndi mkaziyo m'mimba mwace. Pamenepo mliri unaletseka kwa ana a Israyeli.

9 Ndipo akufa nao mliri ndiwo zikwi makumi awiri ndi zinai.

10 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

11 Pinehasi mwana wa Eleazara, mwana wa Aroni wansembe, wabweza kuzaza kwanga pa ana a Israyeli, popeza anacita nsanje ndi nsanje yanga pakati pao, kotero kuti sindinawatha ana a Israyeli m'nsanje yanga.

12 Cifukwa cace nena, Taonani, ndimpatsa iye pangano langa la mtendere;

13 ndipo lidzakhala kwa iye, ndi kwa mbeu zace zakumtsata pangano la unsembe wosatha, popeza anacita nsanje cifukwa ca Mulungu wace, anawacitira ana a Israyeli cowatetezera.

14 Koma dzina la M-israyeli adamuphayo, ndiye amene adamupha pamodzi ndi mkazi Mmidyani, ndiye Zimiri mwana wa Salu, mfumu ya nyumba va makolo mwa Asimeoni.

15 Ndi dzina la mkazi Mmidyani adamuphayo ndiye Kozibi mwana wamkazi wa Zuri; ndiye mkuru wa anthu a nyumba ya makolo m'Midyani.

16 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

17 Sautsa Amidyani ndi kuwakantha;

18 popeza akusautsani ndi manyengo ao amene anakunyengani nao; m'cija ca Peori, ndi ca Kozibi, mwana wamkazi wa kalonga wa ku Midyani, mlongo wao, amene adamupha tsiku la mliri, m'cija ca Peori.

26

1 Ndipo kunali, utatha mliriwo, Yehova ananena ndi Mose ndi Eleazara mwana wa Aroni wansembe, nati,

2 Werenga khamu lonse la ana a Israyeli, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, monga mwa nyumba za makolo ao, onse akuturukira kunkhondo m'Israyeli.

3 Pamenepo Mose ndi Eleazara wansembe ananena nao m'zidikha za Moabu pa Yordano kufupi ku Yeriko, ndi kuti,

4 Awawerenge kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu; monga Yehova anawauza Mose ndi ana a Israyeli, amene adaturuka m'dziko la Aigupto.

5 Rubeni, ndiye woyamba kubadwa wa Israyeli; ana amuna a Rubeni ndiwo: Hanoki, ndiye kholo la banja la Ahanoki; Palu, ndiye kholo la banja la Apalu;

6 Hezeroni, ndiye kholo la banja la Ahezeroni; Karimi, ndiye kholo la banja la Akarimi.

7 Iwo ndiwo mabanja a Arubeni; owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi anai mphambu zitatu kudza mazana asanu ndi awiri mphambu makumi atatu,

8 Mwana wamwamuna wa Palu ndiye Eliyabu.

9 Ndi ana a Eliyabu: Nemueli, ndi Datani ndi Abiramu. Iwo ndiwo Datani ndi Abiramu omwe aja oitanidwa a khamu, amene anatsutsana ndi Mose ndi Aroni mu msonkhano wa Kora, mula anatsutsana ndi Yehova;

10 ndipo dziko linayasama pakamwa pace, ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, pakufa msonkhano uja; muja mote unaononga amuna mazana awiri ndi makumi asanu, nakhala iwo cizindikilo.

11 Koma sanafa ana amuna a Kora.

12 Ana amuna a Simeoni monga mwa mabanja ao ndiwo: Nemueli, ndiye kholo la banja la Anemueli; Yamini, ndiye kholo la banja la Ayamini; Yakini, ndiye kholo la banja la Ayakini;

13 Zera, ndiye kholo la banja la Azera; Sauli, ndiye kholo la banja la Asauli.

14 Iwo ndiwo mabanja a Asimeoni, zikwi makumi awiri mphambu ziwirikudzamazana awiri.

15 Ana amuna a Gadi monga mwa mabanja ao ndiwo: Zefoni, ndiye kholo la banja la Azefoni; Hagi, ndiye kholo la banja la Ahagi; Suni, ndiye kholo la banja la Asuni;

16 Ozini, ndiye kholo la banja la Aozini; Eri, ndiye kholo la banja la Aeri;

17 Arodi, ndiye kholo la banja la Aarodi; Areli, ndiye kholo la banja la Aareli.

18 Iwo ndiwo mabanja a ana a Gadi, monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi anai ndi mazana asanu.

19 Ana amuna a Yuda, ndiwo Eri ndi Onani; ndipo Eri ndi Onani anamwalira m'dziko la Kanani.

20 Ndipo ana a Yuda monga mwa mabanja ao ndiwo: Sela, ndiye kholo la banja la Asela; Perezi, ndiye kholo la banja la Aperezi; Zera, ndiye kholo la banja la Azera.

21 Ndipo ana a Perezi ndiwo: Hezeroni, ndiye kholo la banja la Ahezeroni; Hamuli, ndiye kholo la banja la Ahamuli.

22 Iwo ndiwo mabanja a Yuda monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi asanu ndi awiri mphambu zisanu ndi cimodzi kudza mazana asanu.

23 Ana amuna a Isakara monga mwa mabanja ao ndiwo: Tola, ndiye kholo la banja la Atola; Puva, ndiye kholo la banja la Apuni;

24 Yasubi, ndiye kholo la banja la Ayasubi; Simironi, ndiye kholo la banja la Asimironi.

25 Iwo ndiwo mabanja a Isakara monga mwa owerengedwa ao; zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu zinai kudza mazana atatu.

26 Ana amuna a Zebuloni monga mwa mabanja ao ndiwo: Seredi, ndiye kholo la banja la Aseredi; Eloni, ndiye kholo la banja la Aeloni; Yahaliyeli, ndiye kholo la banja la Ayahaliyeli.

27 Iwo ndiwo mabanja a Zebuloni monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu mazana asanu.

28 Ana amuna a Yosefe monga mwa mabanja ao ndiwo: Manase ndi Efraimu.

29 Ana a Manase ndiwo: Makiri, ndiye kholo la banja la Amakiri; ndipo Makiri anabala Gileadi; ndiye kholo la banja la Agileadi,

30 Ana a Gileadi ndiwo: Yezeri, ndiye kholo la banja la Ayezeri; Heleki, ndiye kholo la banja la Aheleki;

31 ndi Asiriyeli, ndiye kholo la banja la Aasiriyeli; ndi Sekemu, ndiye kholo la banja la Asekemu;

32 ndi Semida, ndiye kholo la banja la Asemida; ndi Heferi, ndiye kholo la banja la Aheferi.

33 Ndipo Tselofekadi mwana wa Heferi analibe ana amuna, koma ana akazi ndiwo; ndipo maina a ana akazi a Tselofekadi ndiwo Mala ndi Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.

34 Iwo ndiwo mabanja ao a Manase; ndipo owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi asanu mphambu ziwiri kudza mazana asanu ndi awiri.

35 Ana amuna a Efraimu monga mwa mabanja ao ndiwo: Sutela, ndiye kholo la banja la Asutela; Bekeri, ndiye kholo la banja la Abekeri; Tahana, ndiye kholo la banja la Atahana.

36 Ndipo mwana wamwamuna wa Sutela ndiye Erani, ndiye kholo la banja la Aerani.

37 Iwo ndiwo mabanja a ana a Efraimu monga mwa owerengedwa ao, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu ziwiri kudza mazana asanu. Iwo ndiwo ana amuna a Yosefe monga mwa mabanja ao.

38 Ana amuna a Benjamini monga mwa mabanja ao ndiwo: Bela, ndiye kholo la banja la Abela; Asibeli, ndiye kholo la banja la Aasibeli; Ahiramu, ndiye kholo la banja la Aahiramu;

39 Sufamu ndiye kholo la banja la Asufamu; Hufamu, ndiye kholo la banja la Ahufamu.

40 Ndipo ana amuna a Bela ndiwo Aridi ndi Namani; Aridi, ndiye kholo la banja la Aaridi; Namani, ndiye kholo la banja la Anamani.

41 Iwo ndiwo ana a Benjamini monga mwa mabanja ao; ndipo owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu kudza mazana asanu ndi limodzi.

42 Mwana wamwamuna wa Dani monga mwa mabanja ace ndiye Suhamu, ndiye kholo la banja la Asuhamu. Iwo ndiwo mabanja a Dani monga mwa mabanja ao.

43 Mabanja aose a Asuhamu monga mwa owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu zinai kudza mazana anai.

44 Ana amuna a Aseri monga mwa mabanja ao ndiwo: Yimna, ndiye kholo la banja la Ayimna; Yisivi, ndiye kholo la banja la Ayisivi; Beriya, ndiye kholo la banja la Aberiya.

45 Ana a Beriya ndiwo: Heberi, ndiye kholo la banja la Aheberi; Malikiyeli, ndiye kholo la banja la Amalikiyeli.

46 Ndipo dzina la mwana wamkazi wa Aseri ndiye Sera.

47 Iwo ndiwo mabanja a ana amuna a Aseri monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi asanu mphambu zitatu kudza mazana anai.

48 Ana amuna a Nafitali monga mwa mabanja ao ndiwo: Yazeli, ndiye kholo la banja la Ayazeli; Guni, ndiye kholo la banja la Aguni;

49 Yezeri, ndiye kholo la banja la Ayezeri; Silemu, ndiye kholo la banja la Asilemu.

50 Iwo ndiwo mabanja a Nafitali, monga mwa mabanja ao; ndipo owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi anai mphambu zisanu kudza mazana anai.

51 Iwo ndiwo owerengedwa ao a ana a Israyeli, zikwi mazana asanu ndi limodzi mphambu cimodzi kudza mazana asanu ndi awiri mphambu makumi atatu.

52 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

53 Dziko ligawikire iwowa monga mwa kuwerenga kwa maina, likhale colowa cao.

54 Ocurukawo, uwacurukitsire colowa cao; ocepawo uwacepetsere colowa cao; ampatse yense colowa cace monga mwa owerengedwa ace.

55 Koma aligawe ndi kucita maere; colowa cao cikhale monga mwa maina a mafuko a makolo ao,

56 Agawire ocuruka ndi ocepa colowa cao monga mwa kucita maere.

57 Ndipo awa ndi owerengedwa ao a Alevi monga mwa mabanja ao: Gerisoni, ndiye kholo la banja la Agerisoni; Kohati, ndiye kholo la banja la Akohati; Merari, ndiye kholo la banja la Amerari.

58 Awa ndi mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, banja la Akohati. Ndipo Kohati anabala Amiramu.

59 Ndipo dzina lace la mkazi wace wa Amiramu ndiye Yokebedi, mwana wamkazi wa Levi, wobadwira Levi m'Aigupto; ndipo iye anambalira Amiramu Aroni ndi Mose, ndi Miriamu mlongo wao.

60 Ndipo Nadabu ndi Abihu, Eleazara ndi ltamara anabadwira Aroni.

61 Koma Nadabu ndi Abihu adafa, muja anabwera nao moto wacilendo pamaso pa Yehova.

62 Ndipo owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi awiri mphambu zitatu, mwamuna yense wa mwezi umodzi ndi mphambu; popeza sanawerengedwa pakati pa ana a Israyeli; cifukwa sanawapatsa colowa mwa ana a Israyeli.

63 Iwo ndiwo amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eleazara wansembe, amene anawerenga ana a Israyeli m'zidikha za Moabu ku Yordano pafupi pa Yeriko.

64 Koma pakati pao panalibe mmodzi wa iwo amene anawerengedwa ndi Mose ndi Aroni wansembe, amene anawerenga ana a Israyeli m'cipululu ca Sinai.

65 Popeza Yehova adanena za iwowa, Adzafatu m'cipululu. Ndipo sanatsalira mmodzi wa iwowa koma Kalebi mwana wa Yefune, ndi Yoswa mwana wa Nuni.

27

1 Pamenepo anayandikiza ana akazi a Tselofekadi mwana wa Heferi, ndiye mwana wa Gileadi, ndiye mwana wa Makiri, ndiye mwana wamwamuna wa Manase, wa mabanja a Manase mwana wa Yosefe; ndipo maina a ana ace akazi ndiwo, Mala, Nowa, Hogila ndi Milika ndi Tiriza.

2 Ndipo anaima pamaso pa Mose, ndi pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa akalonga, ndi khamu lonse, pakhomo pa cihema cokomanako, ndi kuti,

3 Atate wathu adamwalira m'cipululu, ndipo sanakhala iye pakati pa msonkhano wa iwo akusonkhana kutsutsana ndi Yehova, mu msonkhano wa Kora; koma anafera zoipa zace zace; ndipo analibe ana amuna.

4 Licotsedwerenji dzina la atate wathu pakati pa banja lace, popeza alibe mwana wamwamuna? Tipatseni dziko lathu lathu pakati pa abale a atate wathu.

5 Ndipo Mose anapita nao mlandu wao pamaso pa Yehova.

6 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

7 Ana akazi a Tselofekadi anena zaona; uwapatse ndithu colowa cikhale cao cao pakati pa abale a atate wao; nuwalandiritse colowa ca atate wao.

8 Ndipo unene ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Akafa munthu wamwamuna wopanda mwana wamwamuna, colowa cace acilandire mwana wace wamkazi.

9 Ndipo akapanda kukhala naye mwana wamkazi, mupatse abale ace colowa cace.

10 Ndipo akapanda kukhala nao abale, mupatse abale a atate wace colowa cace.

11 Ndipo akapanda abale a atate wace, mupatse wa cibale cace woyandikizana naye wa pfuko lace colowa cace, likhale lace lace; ndipo likhale kwa ana a Israyeli lemba monga Yehova wamuuza Mose.

12 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Kwera m'phiri ili la Abarimu, nupenye dziko limene ndapatsa ana a Israyeli,

13 Utaliona iwenso udzaitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wako, monga anaitanidwa Aroni mbale wako;

14 popeza munapikisana nao mau anga m'cipululu ca Zini, potsutsana nane khamulo, osandipatula Ine pa madziwo pamaso pao. Ndiwo madzi a Meriba m'Kadesi, m'cipululu ca Zini.

15 Ndipo Mose ananena ndi Yehova, nati,

16 Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, aike munthu pa khamulo,

17 wakuturuka pamaso pao, ndi kulowa pamaso pao, wakuwaturutsa ndi kuwalowetsa; kuti khamu la Ambuye lisakhale ngati nkhosa zopanda mbusa.

18 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Utenge Yoswa mwana wa Nuni, ndiye munthu mwa iye muli mzimu, nuike dzanja lako pa iye;

19 numuimike pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse; numlangize pamaso pao.

20 Ndipo umuikirepo ulemerero wako, kuti khamu lonse la ana a Israyeli ammvere.

21 Ndipo aime pamaso pa Eleazara wansembe, amene amfunsire monga mwa ciweruzo ca Urimu pamaso pa Yehova; ponena iye azituruka, ndi ponena iye azilowa, ndi iye ndi ana onse a Israyeli pamodzi naye, ndiwo khamu lonse.

22 Ndipo Mose anacita monga Yehova adamuuza; natenga Yoswa namuimitsa pamaso pa Eleazara wansembe, ndi pamaso pa khamu lonse;

23 namuikira manja ace, namlangiza monga Yehova adanena ndi dzanja la Mose.

28

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Uza ana a Israyeli, nuti nao, Muzisamalira kubwera naco kwa Ine copereka canga, cakudya canga ca nsembe zanga zamoto, ca pfungo lokoma, pa nyengo yace yoikika.

3 Ndipo unene nao, Nsembe yamoto imene muzibwera nayo kwa Yehova ndiyi: ana a nkhosa awiri a caka cimodzi opanda cirema, tsiku ndi tsiku, nsembe yamoto yosalekeza.

4 Mwana wa nkhosa mmodziyo umpereke m'mawa, ndi mwana wa nkhosa winayo umpereke madzulo;

5 ndi limodzi la magawo khumi la efa wa ufa wosalala ukhale nsembe yaufa, wosanganiza ndi limodzi la magawo anai la bini wa mafuta opera.

6 Ndiyo nsembe yopsereza kosalekeza, yoikika ku phiri la Sinai, icite pfungo lokoma, nsembe yamoto ya Yehova.

7 Ndi nsembe yace yothira ya mwana wa nkhosa mmodziyo ndiyo limodzi la magawo anai la bini; m'malo opatulika uthirire Yehova nsembe yothira ya cakumwa colimba.

8 Ndi mwana wa nkhosa winayo umpereke madzulo; monga nsembe yaufa ya m'mawa, ndi nsembe yothira yace, umpereke; ndiyo nsembe yamoto ya pfungo lokoma la Yehova.

9 Ndipo dzuwa la Sabata ana a nkhosa awiri a caka cimodzi, opanda cirema, ndi awiri a magawo khumi a efa wa ufa wosalala, ukhale nsembe yaufa, wosanganiza ndi mafuta, ndi nsembe yace yothira;

10 ndiyo nsembe yopsereza ya dzuwa la Sabata liri lonse, pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yothira.

11 Ndipo poyamba miyezi yanu muzibwera nayo nsembe yopsereza ya Yehova: ng'ombe zamphongo ziwiri, ndi nkhosa yamphongo imodzi, ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri a caka cimodzi opanda cirema;

12 ndi atatu a magawo khumi a efa wa ufa wosalala, ukhale nsembe yaufa, wosanganiza ndi mafuta, ndiwo wa ng'ombe iri yonse; ndi awiri a magawo khumi a ufa wosalala, ukhale nsembe yaufa, wosanganiza ndi mafuta, ndiwo wa nkhosa yamphongo imodziyo;

13 ndi limodzi la magawo khumi la ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa, ndiwo wa mwana wa nkhosa yense; ndiyo nsembe yopsereza ya pfungo lokoma, nsembe yamoto ya. Yehova.

14 Ndipo nsembe zace zothira ndizo: limodzi la magawo khumi la bini wa vinyo ndiwo wa ng'ombe imodzi, ndi limodzi la magawo atatu la hini likhale la nkhosa yamphongo, ndi limodzi la magawo anai a hini likhale la mwana wa nkhosa; ndiyo nsembe yopsereza ya mwezi uli wonse kunena miyezi yonse ya caka.

15 Ndi tonde mmodzi, akhale nsembe yaucimo ya Yehova; aikonze pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yothira.

16 Ndipo mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi, pali paskha wa Yehova.

17 Ndipo tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi uwu pali madyerero; masiku asanu ndi awiri azidya mkate wopanda cotupitsa.

18 Tsiku loyamba pali kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena;

19 koma mubwere nayo nsembe yamoto, nsembe yopsereza ya Yehova; ng'ombe ziwiri zamphongo, ndi nkhosa yamphongo imodzi, ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri a caka cimodzi; akhale kwa inu opanda cirema;

20 ndi nsembe yao ya ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta; mupereke atatu a magawo khumi akhale a ng'ombe, ndi awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo;

21 upereke limodzi la magawo khumi likhale la mwana wa nkhosa mmodzi; uzitero ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri;

22 ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo, yakutetezera inu.

23 Mupereke izi pamodzi ndi nsembe yopsereza ya m'mawa, ndiyo ya nsembe yopsereza kosalekeza.

24 Momwemo mupereke cakudya ca nsembe yamoto ca pfungo lokoma la Yehova, tsiku ndi tsiku, masiku asanu ndi awiri, cakupereka pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yothira.

25 Ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri mukhale nako kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena.

26 Momwemonso tsiku la zipatso zoyamba, pobwera nayo nsembe ya ufa watsopano kwa Yehova, m'madyerero anu a masabata, muzikhala nako kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena.

27 Pamenepo muzipereka nsembe yopsereza ya pfungo lokoma kwa Yehova; ng'ombe zamphongo ziwiri, nkhosa yamphongo imodzi, ana a nkhosa asanu ndi awiri a caka cimodzi;

28 ndi nsembe yace ya ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, atatu a magawo khumi akhale a ng'ombe imodzi, awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo imodzi,

29 limodzi la magawo khumi likhale la mwana wa nkhosa mmodzi, momwemo ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri;

30 tonde mmodzi wakutetezera inu.

31 Mupereke izi pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yaufa, zikhale kwa inu zopanda cirema, ndi nsembe zace zothira.

29

1 Ndipo mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku loyamba la mweziwo, muzikhala nako kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena; likukhalireni inu tsiku lakuliza malipenga.

2 Pamenepo muzipereka nsembeyopsereza ya pfungo lokoma kwa Yehova; ng'ombe imodzi yamphongo, nkhosa yamphongo imodzi, ana a nkhosa asanu ndi awiri a caka cimodzi opanda cirema;

3 ndi nsembe yao yaufa, ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, atatu a magawo khumi akhale a ng'ombeyo, awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo,

4 ndi limodzi la magawo khumi likhale la mwana wa nkhosa mmodzi, momwemo ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri;

5 ndi tonde mmodzi wa nsembe yaucimo, yakutetezera inu;

6 pamodzi ndi nsembe yopsereza ya pamwezi, ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira, monga mwa lemba lace, zikhale za pfungo lokoma, nsembe yamoto ya Yehova.

7 Ndipo tsiku la khumi la mwezi wacisanu ndi ciwiri uwu muzikhala nako kusonkhana kopatulika; pamenepo mudzicepetse; musamagwira nchito;

8 koma mubwere nayo nsembe yopsereza kwa Yehova, ya pfungo lokoma; ng'ombe yamphongo imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, ana a nkhosa asanu ndi awiri a caka cimodzi; akhale kwa inu opanda cirema;

9 ndi nsembe yao ya ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, atatu a magawo khumi akhale a ng'ombe, awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo imodziyo;

10 limodzi la magawo khumi likhale la mwana wa nkhosa mmodzi, momwemo ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri;

11 tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo, pamodzi ndi nsembe yaucimo yotetezera, ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira.

12 Ndipo tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi wacisanu ndi ciwiri muzikhala nako kusonkhana kopatulika; musamacita nchito ya masiku ena, koma mucitire Yehova madyerero masiku asanu ndi awiri;

13 ndipo mubwere nayo nsembe yopsereza, ndiyo nsembe yamoto, ya pfungo lokoma kwa Yehova: ng'ombe zamphongo khumi ndi zitatu, nkhosa zamphongo ziwiri, ana a nkhosa khumi ndi anai, a caka cimodzi, akhale opanda cirema;

14 ndi nsembe yace yaufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, atatu a magawo khumi akhale a ng'ombe imodzi, momwemo nazo ng'ombe khumi ndi zitatuzo, awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo imodzi, momwemo nazo nkhosa zamphongo ziwirizo;

15 ndi limodzi la magawo khumi likhale la mwana wa nkhosa mmodzi, momwemo nao ana a nkhosa khumi ndi anai;

16 ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo; pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, nsembe yace yaufa, ndi nsembe yace yothira.

17 Ndipo tsiku laciwiri muzibwera nazo ng'ombe zamphongo khumi ndi ziwiri, nkhosa zamphongo ziwiri, ana a nkhosa khumi ndi anai a caka cimodzi, opanda cirema;

18 ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira, za ng'ombe, za nkhosa zamphongo, ndi za ana a nkhosa, monga mwa kuwerenga kwace, ndi kutsata lemba lace;

19 ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo; pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira.

20 Ndi tsiku lacitatu ng'ombe khumi ndi imodzi, nkhosa zamphongo ziwiri, ana a nkhosa khumi ndi anai a caka cimodzi opanda cirema;

21 ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira za ng'ombe, za nkhosa zamphongo, ndi za ana a nkhosa monga mwa kuwerenga kwace, ndi kutsata lemba lace;

22 ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo; pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe yace yothira.

23 Ndi tsiku lacinai ng'ombe khumi, nkhosa zamphongo ziwiri, ana a nkhosa khumi ndi anai, a caka cimodzi, opanda cirema;

24 nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira za ng'ombe, za nkhosa zamphongo, ndi za ana a nkhosa, monga mwa kuwerenga kwace, ndi kutsata lemba lace;

25 ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo; pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, nsembe yace yaufa, ndi nsembe yace yothira.

26 Ndi tsiku lacisanu ng'ombe zisanu ndi zinai, nkhosa zamphongo ziwiri, ana a nkhosa khumi ndi anai, a caka cimodzi, opanda cirema;

27 ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira, za ng'ombe, za nkhosa zamphongo, ndi za ana a nkhosa, monga mwa kuwerenga kwace, ndi kutsata lemba lace;

28 ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo; pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe yace yothira.

29 Ndi tsiku lacisanu ndi cimodzi ng'ombe zisanu ndi zitatu, nkhosa zamphongo ziwiri, ana a nkhosa khumi ndi anai, a caka cimodzi, opanda cirema;

30 ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira, za ng'ombe, za nkhosa zamphongo, ndi za ana a nkhosa, monga mwa kuwerenga kwace, ndi kutsata lemba lace;

31 ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo; pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, nsembe yace yaufa, ndi nsembe yace yothira.

32 Ndi tsiku lacisanu ndi ciwiri ng'ombe zisanu ndi ziwiri, nkhosa zamphongo ziwiri, ana a nkhosa khumi ndi anai, a caka cimodzi, opanda cirema;

33 ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira, za ng'ombe, za nkhosa yamphongo, ndi za ana a nkhosa, monga mwa kuwerenga kwace, ndi kutsata lemba lace;

34 ndi tonde mmodzi akhale nsembe yaucimo; pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, nsembe yace yaufa, ndi nsembe yace yothira.

35 Tsiku lacisanu ndi citatu muzikhala nalo tsiku loletsa; musamacita nchito ya masiku ena;

36 koma mubwere nayo nsembe yopsereza ndiyo nsembe yamoto, ya pfungo lokoma kwa Yehova: ng'ombe imodzi, nkhosa yamphongo imodzi, ana a nkhosa asanu ndi awiri, a caka cimodzi, opanda cirema;

37 nsembe yace yaufa, ndi nsembe zace zothira za ng'ombe, za nkhosa zamphongo, ndi za ana a nkhosa, monga mwa kuwerenga kwace, ndi kutsata lemba lace;

38 ndi tonde mmodzi wa nsembe yaucimo; pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yace yaufa, ndi nsembe yace yothira.

39 Izi muzikonzera Yehova mu nyengo zanu zoikika, pamodzi ndi zowinda zanu, ndi zopereka zanu zaufuru, za nsembe zanu zopsereza, ndi za nsembe zanu zaufa, ndi za nsembe zanu zothira, ndi za nsembe zanu zoyamika.

40 Ndipo Mose ananena ndi ana a Israyeli monga mwa zonse Yehova adamuuza Mose.

30

1 Ndipo Mose ananena ndi akuru a mapfuko a ana a Israyeli, nati, Cinthu anacilamulira Yehova ndi ici:

2 Munthu akacitira Yehovacowinda, kapena akalumbira lumbiro ndi kumangira moyo wace codziletsa, asaipse mau ace; azicita monga mwa zonse zoturuka m'kamwa mwace.

3 Ndipo mkazi akacitira Yehova cowinda, nakadzimanga naco codziletsa, pokhala ali m'nyumba ya atate wace, m'unamwali;

4 ndipo atate wace akamva cowinda cace, ndi codziletsa cace anamanga moyo wace naco, koma wakhala naye cete atate wace; pamenepo zowinda zace zonse zidzakhazikika, ndi codziletsa ciri: conse wamanga naco moyo wace cidzakhazikika.

5 Koma atate wace akamletsa tsiku lakumva iye; zowinda zace zonse, ndi zodziletsa zace zonse anamanga nazo moyo wace, sizidzakhazikika; ndipo Yehova adzamkhululukira, popeza atate wace anamletsa.

6 Ndipo akakwatibwa naye mwamuna, pokhala ali nazo zowinda zace, kapena zonena zopanda pace za milomo yace, zimene anamanga nazo moyo wace;

7 nakazimva mwamuna wace, nakakhala naye cete tsiku lakuzimva iye; pamenepo zowinda zace zidzakhazikika, ndi zodziletsa anamanga nazo moyo wace zidzakhazikika.

8 Kama mwamuna wace akamletsa tsiku lakumva iye; pamenepo adzafafaniza cowinda cace anali naco, ndi zonena zopanda pace za milomo yace, zimene anamanga nazo moyo wace; ndipo Yehova adzamkhululukira.

9 Koma cowinda ca mkazi wamasiye, kapena mkazi wocotsedwa, ziti zonse anamanga nazo moyo wace zidzamkhazikikira.

10 Ndipo ngati anawinda m'nyumba ya mwamuna wace, kapena anamanga moyo wace ndi codziletsa ndi kulumbirapo,

11 ndipo mwanuna wace anamva, koma anakhala naye cete osamletsa, pamenepo zowinda zace zonse zidzakhazikika, ndi zodziletsa zonse anamanga nazo moyo wace zidzakhazikika.

12 Koma ngati mwamuna wace anazifafanizadi tsiku lakuzimva iye, zonse zoturuka m'milomo yace kunena za zowinda zace, kapena za codziletsa ca moyo wace sizidzakhazikika; mwamuna wace anazifafaniza; ndipo Yehova adzamkhululukira Iye.

13 Cowinda ciri conse, ndi columbira ciri conse codziletsa cakucepetsa naco moyo, mwamuna wace acikhazikira, kapena mwamuna wace acifafaniza.

14 Koma mwamuna wace akakhala naye cete tsiku ndi tsiku; pamenepo akhazikira zowinda zace zonse, kapena zodziletsa zace zonse, ziri pa iye; wazikhazikitsa, popeza anakhala naye cete tsikuli anazimva iye.

15 Koma akazifafaniza atatha kuzimva; pamenepo adzasenza mphulupulu yace.

16 Awa ndi malemba amene Yehova analamulira Mose, a pakati pa mwamuna ndi mkazi wace, pakati pa atate ndi mwana wace wamkazi, akali namwali, m'nyumba ya atate wace.

31

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Abwezereni cilango Amidyani cifukwa ca ana a Israyeli; utatero udzaitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wako.

3 Ndipo Mose ananena ndi anthu, nati, Adzikonzere ena mwa inu zida za nkhondo, alimbane nao Amidyani, kuwabwezera Amidyani cilango ca Yehova.

4 Muwatume kunkhondo a pfuko limodzi, cikwi cimodzi, a pfuko limodzi cikwi cimodzi, atere mafuko onse a Israyeli.

5 Ndipo anapereka mwa zikwi za Israyeli, a pfuko limodzi cikwi cimodzi, anthu zikwi khumi ndi ziwiri okonzekeratu ndi zankhondo.

6 Ndipo Mose anawatuma a pfuko limodzi cikwi cimodzi, kunkhondo, iwowa ndi Pinehasi mwana wa Eleazara wansembe, kunkhondo, ndi zipangizo zopatulika, ndi malipenga oliza m'dzanja lace.

7 Ndipo anawathira nkhondo Amidyani, monga Yehova adamuuza Mose; nawapha amuna onse.

8 Ndipo anapha mafumu a Amidyani pamodzi ndi ophedwa ao ena; ndiwo Evi, ndi Rekamu, ndi Zuri, ndi Huri, ndi Reba, mafumu asanu a Amidyani; namupha Balamu mwana wa Beori ndi lupanga.

9 Ndipo ana a Israyeli anagwira akazi a Amidyani, ndi ana ang'ono, nafunkha ng'ombe zao zonse, ndi zoweta zao zonse, ndi cuma cao conse.

10 Ndipo anatentha ndi moto midzi yao yonse yokhalamo iwo, ndi zigono zao zonse.

11 Ndipo anapita nazo zofunkha zonse, ndi zakunkhondo zonse, ndizo anthu ndi nyama.

12 Ndipo anadza nao andende, ndi zakunkhondo, ndi zofunkha, kwa Mose, ndi kwa Eleazara wansembe, ndi kwa khamu la ana a Israyeli, kucigono, ku zidikha za Moabu, ziri ku Yordano pafupi pa Yeriko.

13 Ndipo Mose, ndi Eleazara wansembe, ndi akalonga onse a khamulo, anaturuka kukomana nao kunja kwa cigono.

14 Ndipo Mose anakwiya nao akazembe a nkhondoyi, atsogoleri a zikwi, atsogoleri a mazana, akufuma kunkhondo adaithira.

15 Ndipo Mose ananena nao, Kodi mwasunga ndi moyo akazi onse?

16 Taonani, awa analakwitsa ana a Israyeli pa Yehova nilica Peoricija, monga adawapangira Balamu; kotero kuti kunali mliri m'khamu la Yehova.

17 Ndipo tsono iphani amuna onse mwa anawo, iphaninso akazi onse akudziwa mwamuna mogona naye.

18 Koma ana akazi onse osadziwa mwamuna mogona naye, asungeru ndi moyo akhale anu.

19 Ndipo mukhale m'misasa kunja kwa cigono masiku asanu ndi awiri; ali yense adapha munthu, ndi ali yense wakukhudza wophedwa, mudziyeretse tsiku lacitatu ndi lacisanu ndi ciwiri, inu ndi andende anu.

20 Muyeretse zobvala zanu zonse, zipangizo zonse zacikopa, ndi zaomba zonse za ubweya wa mbuzi, ndi zipangizo zonse zamtengo.

21 Ndipo Eleazara wansembe ananena ndi ankhondo adapita kunkhondowo, Lemba la cilamuloco Yehova analamulira Mose ndi ili:

22 Golidi, ndi siliva, mkuwa, citsulo, ndolo ndi mtobvu zokha,

23 zonse zakulola moto, mupititse m'moto, ndipo zidzakhala zoyera; koma muziyeretsenso ndi madzi akusiyanitsa. Koma zonse zosalola moto, muzipititse m'madzi.

24 Ndipo muzitsuke zobvala zanu tsiku lacisanu ndi ciwiri, kuti mukhale oyera; ndipo mutatero mulowe m'cigono.

25 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

26 Werengani zakunkhondo, ndizo anthu, ndi zoweta, iwe; ndi Eleazara wansembe, ndi akuru a nyumba za makolo za khamulo;

27 nugawe zakunkhondo pawiri; pakati pa othira nkhondo amene anaturuka kunkhondo, ndi khamu lonse.

28 Ndipo usonkhetse anthu ankhondo akuturuka kunkhondo apereke kwa Yehova; munthu mmodzi mwa anthu mazana asanu, mwa ng'ombe, mwa aburu, mwa nkhosa ndi mbuzi, momwemo.

29 Uzitenge ku gawo lao, ndi kuzipereka kwa Eleazara wansembe, zikhale nsembe yokweza ya Yehova.

30 Ndipo ku gawo la ana a Israyeli utenge munthu mmodzi mwa anthu makumi asanu, mwa ng'ombe, mwa aburu, mwa nkhosa ndi mbuzi, mwa zoweta zonse, momwemo; nuzipereke kwa Alevi, akusunga udikiro wa kacisi wa Yehova.

31 Ndipo Mose ndi Eleazara wansembe anacita monga Yehova anamuuza Mose.

32 Ndipo zakunkhondo, zotsalira zofunkha zonse adazifunkha ankhondowa, ndizo nkhosa zikwi mazana asanu ndi limodzi mphambu zikwi makumi asanu ndi awiri kudza zisanu,

33 ndi ng'ombe zikwi makumi asanu ndi awiri mphambu ziwiri,

34 ndi aburu zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu cimodzi,

35 ndi anthu, ndiwo akazi osadziwa mwamuna mogona naye, onse pamodzi zikwi makumi atatu ndi ziwiri.

36 Ndipo limodzi la magawo awiri, ndilo gawo la iwo adaturuka kunkhondo, linafikira nkhosa zikwi mazana atatu mphambu makumi atatu kudza zisanu ndi ziwiri mphambu mazana asanu.

37 Ndi msonkho wa Yehova wankhosa ndiwo mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi awiri mphambu zisanu.

38 Ndipo ng'ombe zidafikira zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi cimodzi; pamenepo msonkho wa Yehova ndiwo makumi asanu ndi awiri mphambu ziwiri.

39 Ndipo aburu anafikira zikwi makumi atatu ndi mazana asanu; pamenepo msonkho wa Yehova ndiwo makumi asanu ndi limodzi mphambu mmodzi.

40 Ndipo anthu anafikira zikwi khumi ndi zisanu ndi cimodzi; pamenepo msonkho wa Yehova ndiwo anthu makumi atatu mphambu awiri.

41 Ndipo Mose anapereka zamsonkhozo, ndizo nsembe yokweza ya Yehova, kwa Eleazara wansembe, monga Yehova adamuuza Mose.

42 Ndipo kunena za gawo la ana a Israyeli, limene Mose adalicotsa kwa anthu ocita nkhondowo,

43 (ndipo gawo la khamulo ndilo nkhosa zikwi mazana atatu mphambu makumi atatu kudza zisanu ndi ziwiri mphambu mazana asanu,

44 ndi ng'ombe zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi cimodzi,

45 ndi aburu zikwi makumi atatu ndi mazana asanu,

46 ndi anthu zikwi khumi ndi zisanu ndi cimodzi,)

47 mwa gawolo la ana a Israyeli Mose anatenga munthu mmodzi mwa makumi asanu, ndi zoweta momwemo, nazipereka kwa Alevi, akusunga udikiro wa kacisi wa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

48 Pamenepo akazembe a pa ankhondo zikwi, atsogoleri a zikwi, ndi atsogoleri a mazana, anayandikiza kwa Mose;

49 nati kwa Mose, Atumiki anu anawerenga ankhondo tinali nao, ndipo sanasowa munthu mmodzi wa ife.

50 Ndipo tabwera naco copereka ca Yehova, yense cimene anacipeza, zokometsera zagolidi, unyolo, zikwinjiri, mphete zosindikizira, nsapule, ndi mkanda, kucita cotetezera moyo wathu pamaso pa Yehova.

51 Ndipo Mose ndi Eleazara wansembe analandira golidiyo kwa iwowo, ndizo zokometsera zonse zokonzeka.

52 Ndipo golidi yense wa nsembe yokweza ya Yehova amene anapereka kwa Yehova, wofuma kwa atsogoleri a zikwi, ndi atsogoleri a mazana, ndiwo masekeli zikwi khumi ndi zisanu ndi cimodzi mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu.

53 Popeza wankhondo yense anadzifunkhira yekha.

54 Ndipo Mose ndi Eleazara wansembe analandira golidi kwa akuru a zikwi ndi a mazana, nalowa naye ku cihema cokomanako, cikumbutso ca ana a Israyeli pamaso pa Yehova.

32

1 Koma ana a Rubeni ndi ana a Gadi anali nazo zoweta zambirimbiri; ndipo anapenyerera dziko la Yazeri, ndi dziko la Gileadi, ndipo taonani, malowo ndiwo malo a zoweta.

2 Pamenepo ana a Gadi ndi ana a Rubeni anadza nanena ndi Mose, ndi Eleazara wansembe, ndi akalonga a khamulo, nati,

3 Ataroti, ndi Diboni, ndi Yazeri, ndi Nimra, ndi Heseboni, ndi Eleyali, ndi Sebamu, ndi Nebo, ndi Beoni,

4 dzikoli Yehova analikantha pamaso pa khamu la Israyeli, ndilo dziko la zoweta ndipo anyamata anu ali nazo zoweta.

5 Ndipo anati, Ngati tapeza ufulu pamaso panu, mupatse anyamata anu dziko ili likhale lao lao; tisaoloke Yordano.

6 Ndipo Mose anati kwa ana a Gadi ndi ana a Rubeni, Kodi abale anu apite kunkhondo, ndi inu mukhale pansi kuno?

7 Ndipo mufoketseranji mtima wa ana a Israyeli kuti asaoloke ndi kulowa dzikoli Yehova anawapatsa?

8 Anatero makolo anu, muja ndinawatumiza acoke ku Kadesi Barinea kukaona dziko.

9 Popeza atakwera kumka ku cigwa ca Esikolo, naona dziko, anafoketsa mtima wa ana a Israyeli, kuti asalowe dzikoli Yehova adawapatsa.

10 Ndipo Yehova anapsa mtima tsiku lija, nalumbira iye, nati,

11 Anthu adakwerawo kuturuka m'Aigupto, kuyambira wa zaka makumi awiri ndi mphambu sadzaona dziko limene ndinalumbirira Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo; popeza sananditsata Ine ndi mtima wonse;

12 koma Kalebi mwana wa Yefune, Mkenizi, ndi Yoswa mwana wa Nuni ndiwo; popeza anatsata Yehova ndi mtima wonse.

13 Ndipo Yehova anapsa mtima pa Israyeli, nawayendetsa-yendetsa m'cipululu zaka makumi anai, kufikira utatha mbadwo wonsewo udacita coipa pamaso pa Yehova.

14 Ndipo taonani, mwauka m'malo mwa makolo anu, gulu la anthu ocimwa, kuonjezanso mkwiyo waukali wa Yehova pa Israyeli,

15 Pakuti mukabwerera m'mbuyo kusamtsata iye, adzawasiyanso m'cipululu, ndipo mudzaononga anthu awa onse.

16 Ndipo anayandikiza, nati, Tidzamangira zoweta zathu makola kuno, ndi ana athu midzi; koma ife tidzakhala okonzeka ndi kufulumira pamaso pa ana a Israyeli, kufikira tidawafikitsa kumalo kwao;

17 ndi ang'ono athu adzakhala m'midzi ya malinga cifukwa ca okhala m'dzikomo.

18 Sitidzabwerera kwathu, kufikira ana a Israyeli atalandira yense colowa cace.

19 Pakuti sitidzalandira pamodzi nao tsidya la Yordano, ndi m'tsogolo mwace; popeza colowa cathu tacilandira tsidya lino la Yordano kum'mawa.

20 Ndipo Mose anati nao, Ngati mudzacita ici, ndi kudzikonza kunkhondo pamaso pa Yehova,

21 ndi kuoloka Yordano pamaso pa Yehova okonzeka onse mwa inu, kufikira atapitikitsa adani ace pamaso pace,

22 ndi dziko lagonjera Yehova; mutatero mudzabwerere, ndi kukhala osacimwira Yehova ndi Israyeli; ndipo dziko ili lidzakhala lanu lanu pamaso pa Yehova.

23 Koma mukapanda kutero, taonani, mwacimwira Yehova; ndipo zindikirani kuti cimo lanu lidzakupezani.

24 Dzimangireni midzi ya ana anu, ndi makola a zoweta zanu; ndipo muzicite zoturuka m'kamwa mwanu.

25 Ndipo ana a Gadi ndi ana a Rubeni ananena ndi Mose, nati, Anyamata anu adzacita monga mbuyanga alamulira.

26 Ana athu, akazi athu, zoweta zathu, ndi ng'ombe zathu zonse, zidzakhala komweko m'midzi ya ku Gileadi;

27 koma anyamata anu adzaoloka, yense wokonzekera ndi zankhondo pamaso pa Yehova kunkhondo, monga wanena mbuyanga.

28 Pamenepo Mose anamuuza Eleazara wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni, ndi akuru a makolo a mapfuko a ana a Israyeli za iwo.

29 Ndipo Mose anati kwa iwo, Ngati ana a Gadi ndi ana a Rubeni aoloka nanu Yordano, yense wokonzekera ndi zankhondo pamaso pa Yehova, ndi dziko lagonjera inu; pamenepo muwapatse dziko la Gileadi likhale lao lao;

30 koma akapanda kuoloka nanu okonzeka, akhale nao maiko ao ao pakati pa inu m'dziko la Kanani.

31 Ndipo ana a Gadi ndi ana a Rubeni anayankha, nati, Monga Yehova anati kwa anyamata anu momwemo tidzacita.

32 Tidzaoloka okonzeka pamaso pa Yehova ku dziko la Kanani, koma colowa cathu cathu cikhale tsidya lino la Yordano.

33 Ndipo Mose anawapatsa, ndiwo ana a Gadi, ndi ana a Rubeni ndi pfuko la hafu la Manase mwana wa Yosefe, dziko la Sihoni mfumu ya Aamori, ndi dziko la Ogi mfumu ya Basana, dzikoli ndi midzi yace m'malire mwao, ndiyo midzi ya dziko lozungulirako,

34 Ndipo ana a Gadi anamanga Diboni, ndi Ataroti, ndi Aroeri;

35 Ataroti Sofani, Yazeri, ndi Yogebeha;

36 ndi Beti Nimira, ndi Beti Harani: midzi ya m'malinga, ndi makola a zoweta.

37 Ndipo ana a Rubeni anamanga Hesiboni, ndi Eleyali, ndi Kiriyataimu;

38 ndi Nebo, ndi Baala Meoni (nasintha maina ao), ndi Sibima; ndipo anaicha midzi adaimanga ndi maina ena.

39 Ndipo ana a Makiri mwana wa Manase anamka ku Gileadi, naulanda, napitikitsa Aamori anali m'mwemo.

40 Ndipo Mose anapatsa Makiri mwana wa Manase Gileadi; ndipo anakhala m'menemo.

41 Ndipo Yairi mwana wa Manase anamka nalanda midzi yao, naicha Havoti Yairi. Ndipo Noba anamka nalanda Kenati, ndi miraga yace, naucha Noba, dzina lace.

33

1 Maulendo a ana a Israyeli amene anaturuka m'dziko la Aigupto monga mwa makamu ao, ndi dzanja la Mose ndi Aroni, ndi awa.

2 Ndipo Mose analembera maturukidwe ao monga mwa maulendo ao, monga mwa mau a Yehova; ndipo maulendo ao ndi awa monga mwa maturukidwe ao.

3 Ndipo anacokera ku Ramese mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi woyamba; atacita Paskha m'mawa mwace ana a Israyeli, anaturuka ndi dzanja lokwezeka pamaso pa Aaigupto onse,

4 pamene Aaigupto ailalikuika oyamba kubadwa ao onse, amene Yehova adawakantha; Yehova adaweruzanso milungu yao.

5 Ndipo ana a Israyeli macokera ku Ramese, nayenda namanga ku Sukoti.

6 Nacokera ku Sukoti, nayenda namanga m'Etamu, ndiko ku malekezero a cipululu.

7 Ndipo anacokera ku Etamu, nayenda nabwerera ku Pihahiroti, ndiko kutsogolo kwace kwa Baala Zefoni; namanga iwo patsogolo pa Migidoli.

8 Ndipo anacokera ku Pihahiroti, naoloka pakati pa nyanja nalowa m'cipululu; nayenda ulendo wa masiku atatu m'cipululu ca Etamu, namanga m'Mara.

9 Ndipo anacokera ku Mara, nayenda nafika ku Elimu, ku Elimu ndiko kuli akasupe khumi ndi awiri a madzi, ndi akanjedza makumi asanu ndi awiri; namanga iwo komweko.

10 Ndipo anacokera ku Elimu, nayenda namanga ku Nyanja Yofiira.

11 Nacokera ku Nyanja Yofiira, nayenda namanga m'cipululu ca Sini.

12 Nacokera ku cipululu ca Sini, nayenda namanga m'Dofika.

13 Nacokera ku Dofika, nayenda namanga m'Alusi.

14 Nacokera ku Alusi, nayenda namanga m'Refidimu; kumeneko kunalibe madzi kuti anthu amwe.

15 Ndipo anacokera ku Refidimu, nayenda namanga m'cipululu ca Sinai.

16 Nacokera ku cipululu ca Sinai, nayenda namanga m'Kibiroti Hatava.

17 Nacokera ku Kibiroti Hatava, nayenda namanga m'Hazeroti.

18 Nacokera ku Hazeroti, nayenda namanga m'Ritima.

19 Nacokera ku Ritima, nayenda namanga m'Rimoni Perezi.

20 Nacokera ku Rimoni Perezi, nayenda namanga m'Libina.

21 Nacokera ku Libina, nayenda namanga m'Risa.

22 Nacokera ku Risa, nayenda namanga m'Kehelata.

23 Nacokera ku Kehelata, nayenda namanga m'phiri la Saferi.

24 Nacokera ku phiri la Saferi, nayenda namanga n'Harada.

25 Nacokera ku Harada, nayenda namanga m'Makeloti.

26 Nacokera ku Makeloti, nayenda namanga m'Tahata.

27 Nacokera ku Tahata, nayenda namanga m'Tara.

28 Nacokera ku Tara, nayenda namanga m'Mitika.

29 Nacokera ku Mitika, nayenda namanga m'Hasimona.

30 Nacokera ku Hasimona, nayenda namanga m'Moseroto.

31 Nacokera ku Moseroto, nayenda namanga m'Bene Yaakana.

32 Nacokera ku Bene Yaakana, nayenda namanga m'Hori Hagidigadi.

33 Nacokera ku Hori Hagidigadi, nayenda namanga m'Yotibata.

34 Nacokera ku Yotibata, nayenda namanga m'Abirona.

35 Nacokera ku Abirona, nayenda namanga m'Ezioni Geberi.

36 Nacokera ku Ezioni Geberi, nayenda namanga m'cipululu ca Zini (ndiko Kadesi).

37 Nacokera ku Kadesi, nayenda namanga m'phiri la Hori, ku malekezero a dziko la Edomu.

38 Ndipo Aroni wansembe anakwera m'phiri la Hori pa mau a Yehova, nafa komweko, ataturuka ana a Israyeli m'dziko la Aigupto zaka makumi anai, mwezi wacisanu, tsiku loyamba la mwezi.

39 Ndipo Aroni ndiye wa zaka zana limodzi mphambu makumi awiri kudza zitatu pakufa iye m'phiri la Hori.

40 Ndipo Mkanani, mfumu ya Aradi, wakukhala kumwela m'dziko la Kanani, anamva za kudza kwao kwa ana a Israyeli.

41 Ndipo anacokera ku phiri la Hori, nayenda namanga m'Tsalimona.

42 Nacokera ku Tsalimona, nayenda namanga m'Punoni.

43 Nacokera ku Punoni, nayenda namanga m'Oboti.

44 Nacokera ku Oboti, nayenda namanga m'iye Abarimu, m'malire a Moabu.

45 Nacokera ku lyimu, nayenda namanga m'Diboni Gadi.

46 Nacokera ku Diboni Gadi, nayenda namanga m'Alimoni Diblataimu.

47 Nacokera ku Alimoni Diblataimu, nayenda namanga m'mapiri a Abarimu, cakuno ca Nebo.

48 Nacokera ku mapiri a Abarimu, nayenda namanga m'zidikhaza Moabu pa Yordano ku Yeriko,

49 Ndipo anamanga pa Yordano, kuyambira ku Beti Yesimoti kufikira ku Abeli Sitimu m'zidikha za Moabu.

50 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'zidikha za Moabu pa YordaBaku Yeriko, nati,

51 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mutaoloka Yordano kulowa m'dziko la Kanani,

52 mupitikitse onse okhala m'dzikopamaso panu, ndi kuononga mafano ao onse a miyala, ndi kuononga mafano ao onse oyenga, ndi kupasula misanje yao yonse;

53 ndipo mulande dziko, ndi kukhala m'mwemo, pakuti ndinakupatsani inu dzikoli likhale lanu lanu.

54 Ndipo mulandire dzikoli ndi kucita maere monga mwa mabanja anu; colowa cao cicurukire ocurukawo, colowa cao cicepere ocepawo; kumene maere amgwera munthu, kumeneko nkwace; mulandire colowa canu monga mwa mapfuko a makolo anu.

55 Koma mukapanda kupitikitsa okhala m'dziko pamaso panu, pamenepo iwo amene muwalola atsale adzakhala ngati zotwikira m'maso mwanu, ndi minga m'mbali zanu, nadzakubvutani m'dziko limene mukhalamo.

56 Ndipo kudzakhala kuti monga ndinayesa kucitira iwowa, ndidzakucitirani inu.

34

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Uza ana Israyeli, nunene nao, Mutalowa a m'dziko la Kanani, ndilo dziko logwera inu, likhale colowa canu, dziko ija Kanani monga mwa malire ace,

3 dera lanu la kumwela lidzakhala locokera ku cipululu ca Zini, kutsata m'mphepete mwa Edomu, ndi malire anu a kumwela adzakhala ocokera ku malekezero a Nyanja ya Mcere kum'mawa;

4 ndi malire anu adzapinda kucokera kumwela kumka pokwera Akrabimu, ndi kupitirira ku Zini; ndi kuturuka kwace adzacokera kumwela ku Kadesi Barinea, nadzaturuka kumka ku Hazara Adara, ndi kupita kumka ku Azimoni;

5 ndipo malirewo adzapinda ku Azimoni kumka ku mtsinje wa Aigupto, ndi kuturuka kwao adzaturuka kunyanja.

6 Kunena za malire a kumadzulo, nyanja yaikuru ndiyo malire anu; ndiyo malire anu a kumadzulo.

7 Malire anu a kumpoto ndiwo: kuyambira ku nyanja yaikuru mulinge ku phiri la Hori:

8 kucokera ku phiri la Hori mulinge polowera Hamati; ndipo kuturuka kwace kwa malire kudzakhala ku Zedadi.

9 Ndipo malirewo adzaturuka kumka ku Zifironi, ndi kuturuka kwace kudzakhala ku Hazara Enani; ndiwo malire anu a kumpoto.

10 Ndipo mudzilembere malire a kum'mawa ocokera ku Hazara Enani kumka ku Sefamu;

11 ndi malire adzatsika ku Sefamu kumka ku Ribala, kum'mawa kwa Ayina; ndipo malire adzatsika, nadzafikira mbali ya nyanja ya Kinereti kum'mawa,

12 ndi malire adzatsika ku Yordano, ndi kuturuka kwace kudzakhala ku Nyanja ya Mcere; ili ndili dziko lanu monga mwa malire ace polizinga.

13 Ndipo Mose anauza ana a Israyeli, nati, Ili ndi dzikoli mudzalandira ndi kucita maere, limene Yehova analamulira awapatse mapfuko asanu ndi anai ndi hafu;

14 popeza pfuko la ana a Rubeni monga mwa nyumba za makolo ao, ndi pfuko la ana a Gadi monga mwa nyumba za makolo ao, adalandira, ndi pfuko la hafu la Manase lalandira colowa cao;

15 mapfuko awiriwa ndi hafu adalandira colowa cao tsidya lija la Yordano ku Yeriko, kum'mawa, koturukira dzuwa.

16 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

17 Maina a amunawo adzakugawirani dziko likhale colowa canu, ndi awa: Eleazara wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni.

18 Muwatengenso akalonga, kalonga mmodzi ku pfuko limodzi, agawe dziko likhale colowa cao.

19 Maina a amunawo ndiwo: wa pfuko la Yuda, Kalebi mwana wa Yefune.

20 Wa pfuko la ana a Simeoni, Semuyeli mwana wa Amihudi.

21 Wa pfuko la Benjamini, Elidadi mwana wa Kisiloni.

22 Wa pfuko la ana a Dani, kalonga Buki mwana wa Yogili.

23 Wa ana a Yosefe; wa pfuko la ana a Manase, kalonga Haniyeli mwana wa Efodi.

24 Wa pfuko la ana a Efraimu, kalonga Kemuyeli mwana wa Sipitana.

25 Wa pfuko la ana a Zebuloni, kalonga Elisafana mwana wa Paranaki.

26 Wa pfuko la ana a Isakara, kalonga Palitiyeli mwana wa Azana.

27 Wa pfuko la ana a Aseri, kalonga Ahihudi mwana wa Selomi.

28 Wa pfuko la ana a Nafitali, kalonga Pedaheli mwana wa Amihudi.

29 Iwo ndiwo amene Yehova analamulira agawire ana a Israyeli colowa cao m'dziko la Kanani.

35

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'zidikha za Moabu, pa Yordano, ku Yeriko, ndi kuti,

2 Uza ana a Israyeli, kuti apatseko Alevi colowa cao cao, midzi yokhalamo; muwapatsenso Alevi mabusa akuzungulira midzi.

3 Ndipo midzi ndiyo yokhalamo iwowa; ndi mabusa akhale a ng'ombe zao, ndi zoweta zao, inde nyama zao zonse.

4 Ndipo mabusa a midziyo, imene muipereke kwa Alevi ndiwo a mikono cikwi cimodzi kuyambira kulinga kufikira kunja.

5 Ndipo muyese kunja kwa mudzi, mbali ya kum'mawa mikono zikwi ziwiri, ndi mbali ya kumwela mikono zikwi ziwiri, ndi mbali ya kumadzulo mikono zikwi ziwiri, ndi mbali ya kumpoto mikono zikwi ziwiri; ndi mudziwo pakati; ndiwo mabusa a kumidzi.

6 Ndipo midziyo muipereke kwa Alevi ndiyd midzi ija isanu ndi umodzi yopulumukirako; imene muipereke kuti wakupha mnzace athawireko; ndipo pamodzi ndi iyi muperekenso midzi makumi anai ndi iwiri.

7 Midzi yonse muipereke kwa Alevi ndiyo midzi makumi anai ndi isanu ndi itatu, iyo pamodzi ndi mabusa ao.

8 Ndipo kunena za midziyo muiperekeyo yao yao ya ana a Israyeli, okhala nayo yambiri mutengeko yambiri; okhala nayo pang'ono mutengeko pang'ono; onse operekako midzi yao kwa Alevi monga mwa colowa cao adacilandira.

9 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

10 Nenandi ana a Israyeli, nuti nao, Pakuoloka inu Yordano kulowa m'dziko la Kanani,

11 muikire midzi ikukhalireni midzi yopulumukirako; kuti wakupha mnzace wosati dala athawireko.

12 Ndipo midziyo ikukhalireni yakupulumuka wolipsa; kuti wakupha mnzace asafe, kufikira ataima pamaso pa msonkhano amweruze.

13 Ndipo midziyo muipereke ikukhalireni midzi isanu ndi umodzi yopulumukirako.

14 Mupereke midzi itatu tsidya lino la Yordano, ndi midzi itatu mupereke m'dziko la Kanani, ndiyo yopulumukirako.

15 Midzi isanu ndi umodzi imene ndiyo yopulumukirako ana a Israyeli, ndi mlendo, ndi wokhala pakati pao; kuti ali yense adamupha munthu osati dala athawireko.

16 Koma akamkantha ndi cipangizo cacitsulo, kuti wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.

17 Kapena akamkantha m'dzanja muli mwala, wakufetsa munthu, ndipo wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.

18 Kapena akamkantha m'dzanja muli cipangizo camtengo, cakufetsa munthu, ndipo wafa, ndiye wakupha munthu; wakupha munthu nayenso amuphe ndithu.

19 Wolipsa mwazi mwini wace aphe wakupha munthuyo; pakumkumika amuphe,

20 Ndipo akampyoza momkwiyira, kapena kumponyera kanthu momlalira, kuti wafa;

21 kapena kumpanda ndi dzanja lace momuda, kuti wafa, womkanthayo nayenso amuphe ndithu; ndiye wakupha munthu; wolipsa mwazi aphe wakupha munthuyo pomkumika.

22 Koma akampyoza modzidzimuka, osamuda, kapena kumponyera kanthu osamialira,

23 kapena kumponyera mwala wakufetsa munthu, osamuona, namgwetsera uwu, kuti wafa, koma sindiye mdani wace, kapena womfunira coipa;

24 pamenepo msonkhano uziweruza pakati pa wokantha mnzaceyo ndi wolipsa mwaziyo monga mwa maweruzo awa;

25 ndipo msonkhano umlanditse wakupha munthu m'dzanja la wolipsa mwazi, ndi msonkhanowo umbwezere ku mudzi wace wopulumukirako, kumene adathawirako; ndipo azikhalamo kufikira atafa mkulu wa ansembe wodzozedwa ndi mafuta opatulika.

26 Koma wakupha munthu akaturuka nthawi iri yonse kulumpha malire a mudzi wace wopulumukirako kumene anathawirako;

27 nakampeza wolipsa mwazi kunja kwa malire a mudzi wace wothawirako, ndipo wolipsa mwazi akapha wakupha munthu, alibe kucimwira mwazi;

28 popeza wakupha munthu akadakhala m'mudzi wace wopulumukirako kufikira atafa mkulu wa ansembe; koma atafa mkulu wa ansembe wakupha munthuyo abwere ku dziko lace lace.

29 Ndipo izi zikhale kwa inu lemba la ciweruzo mwa mibadwo yanu, m'nyumba zanu zonse.

30 Ali yense wakantha munthu, wakupha munthuyo aziphedwa pakamwa pa mboni; koma mboni ya munthu mmodzi isafikire kuti munthu afe.

31 Musamalandira dipo lakuombola moyo wa iye adapha munthu, naparamula imfa; koma aziphedwa ndithu.

32 Musamalandira dipo lakuombola iye amene adathawira ku mudzi wace wopulumukirako, kuti abwerenso kukhala m'dziko, kufikira atafa wansembe.

33 Ndipo musamaipsa dziko muli m'mwemo; popeza mwazi uipsa dziko; pakuti kulibe kutetezera dziko cifukwa ca mwazi anaukhetsa m'mwemo, koma ndi mwazi wa iye anaukhetsa ndiwo.

34 Usamadetsa dziko ukhala m'mwemo, limene ndikhalitsa pakati pace; popeza Ine Yehova ndikhalitsa pakati pa ana a Israyeli.

36

1 Ndipo akuru a makolo a mabanja a ana a Gileadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase, wa mabanja a ana a Yosefe, anayandikiza, nanena pamaso pa Mose, ndi pamaso pa akalonga, ndiwo akuru a makolo a ana a Israyeli;

2 nati, Yehova analamulira mbuye wanga mupatse ana a Israyeli dzikoli mocita maere likhale colowa cao; ndipo Yehova analamulira mbuye wathu mupatse ana ace akazi colowa ca Tselofekadi mbale wathu.

3 Ndipo akakwatibwa nao ana amuna a mapfuko ena a ana a Israyeli, acicotse colowa cao ku colowa ca makolo athu, nacionjeze ku colowa ca pfuko limene adzakhalako; cotero acicotse ku maere a colowa cathu.

4 Ndipo pofika caka coliza ca ana a Israyeli adzaphatikiza colowa cao ku colowa ca pfuko limene akhalako; cotero adzacotsa colowa cao ku colowa ca pfuko la makolo athu.

5 Ndipo Mose analamulira ana a Israyeli monga mwa mau a Yehova, nati, Pfuko la ana a Yosefe linena zaona.

6 Colamulira Yehova za ana akazi a Tselofekadi ndi ici, kuti, Akwatibwe nao amene afuna eni ace; komatu akwatibwe nao a banja la pfuko la makolo ao okha okha.

7 Motero colowa ca ana a Israyeli sicidzamka m'pfuko m'pfuko; popeza ana a Israyeli adzamamatira yense ku colowa ca pfuko la makolo ace.

8 Ndipo mwana wamkazi yense wa mapfuko a ana a Israyeli, wakukhala naco colowa, akwatibwe ndi wina wa banja la pfuko la kholo lace, kuti ana a Israyeli akhale naco yense colowa ca makolo ace.

9 Motero colowa ca ana a Israyeli sicidzamka m'pfuko m'pfuko, pakuti mapfuko a ana a Israyeli adzamamatira lonse ku colowa cace cace.

10 Monga Yehova adalamulira Mose, momwemo ana akazi a Tselofekadi anacita;

11 popeza Mala, Tiriza, ndi Hogila, ndi Milika, ndi Nowa, ana akazi a Tselofekadi, anakwatibwa ndi ana amuna a abale a atate wao.

12 Anakwatibwa mwa mabanja a ana a Manase mwana wa Yosefe; ndipo colowa cao dnakhala m'pfuko la banja la atate wao.

13 Awa ndi malamulo ndi maweruzo, amene Yehova analamulira ana a Israyeli ndi dzanja la Mose m'zidikha za Moabu pa Yordano ku Yeriko.