1

1 YAKOBO, kapolo wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Kristu, kwa mafuko khumi ndi awiri a m'cibalaliko: ndikulankhulani.

2 Muciyese cimwemwe cokha, abale anga, m'mene mukugwa m'mayesero a mitundu mitundu;

3 pozindikira kuti ciyesedwe ca cikhulupiriro canu cicita cipiriro.

4 Koma cipiriro cikhale nayo nchito yace yangwiro, kuti mukakhale angwiro ndi opanda cirema, osasowa kanthu konse.

5 Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye,

6 Koma apemphe ndi cikhulupiriro, wosakayika konse; pakuti wokayikayo afanana ndi pfunde la nyanja lotengeka ndi mphepo ndi kuwinduka nayo.

7 Pakuti asayese munthu uyu kuti adzalandira kanthu kwa Ambuye;

8 munthu wa mitima iwiri akhala wosinkhasinkha pa njira zace zonse.

9 Koma mbale woluluka adzitamandire pa ukulu wace;

10 pakuti adzapita monga duwa la udzu,

11 Pakuti laturuka dzuwa ndi kutentha kwace, ndipo laumitsa udzu; ndipo lathothoka duwa lace, ndi ukoma wa maonekedwe ace waonongeka; koteronso wacuma adzafota m'mayendedwe ace.

12 Wodala munthu wakupirira poyesedwa; pakuti pamene wabvomerezeka, adzalandira korona wa moyo, amene Ambuye adalonjezera iwo akumkonda iye.

13 Munthu poyesedwa, asanena, Ndiyesedwa ndi Mulungu; pakuti Mulungu sakhoza kuyesedwa ndi zoipa, ndipo iye mwini sayesa munthu:

14 koma munthu ali yense ayesedwa pamene cilakolako cace ca iye mwini cimkokera, nicimnyenga.

15 Pamenepo cilakolakoco citaima, cibala ucimo; ndipo ucimo, utakula msinkhu, ubala imfa.

16 Musanyengedwe, abale anga okondedwa.

17 Mphatso iri yonse yabwino, ndi cininkho ciri conse cangwiro zicokera Kumwamba, zotsika kwa Atate wa mauniko, amene alibe cisanduliko, kapena mthunzi wa citembenukiro.

18 Mwa cifuniro cace mwini anatibala ife ndi mau a coonadi, kuti tikhale ife ngati zipatso zoundukula za zolengedwa zace.

19 Mudziwa, abale anga okondedwa, kuti munthu ali yense akhale wochera khutu, wodekha polankhula, wodekha pakupsa mtima.

20 Pakuti mkwiyo wa munthu sucita cilungamo ca Mulungu.

21 Mwa ici, mutabvula cinyanso conse ndi cisefukiro ca coipa, landirani ndi cifatso mau ookedwa mwa inu, okhoza kupulumutsa moyo wanu.

22 Khalani akucita mau, osati akumva okha, ndi kudzinyenga nokha.

23 Pakuti ngati munthu ali wakumva mau wosati wakucita, iyeyu afanana ndi munthu wakuyang'anira nkhope yace ya cibadwidwe cace m'kalirole;

24 pakuti wadziyang'anira yekha nacoka, naiwala pompaja nali wotani.

25 Koma iye wakupenyerera m'lamulo langwiro, ndilo laufulu, natero cipenyerere, ameneyo, posakhala wakumva wakuiwala, komatu wakucita nchito, adzakhala wodala m'kucita kwace.

26 Ngati wina adziyesera ali wopembedza Mulungu, ndiye wosamanga lilime lace, koma adzinyenga mtima wace, kupembedza kwace kwa munthuyu nkopanda pace.

27 Mapembedzedwe oyera ndi osadetsa pamaso pa Mulungu ndi Atate ndiwo: z kuceza ndi ana amasiye ndi akazi amasiye m'cisautso cao, ndi 1 kudzisungira mwini wosacitidwa mawanga ndi dziko lapansi.

2

1 Abate anga, musakhale naco cikhulupiriro ca Ambuye wathu Yesu Kristu, Ambuye wa ulemerero, ndi kusamala maonekedwe.

2 Pakuti akalowa m'sunagoge mwanu munthu wobvala mphete yagolidi, ndi cobvala cokometsetsa, ndipo akalowanso munthu wosauka ndi cobvala codetsa:

3 ndipo mukapenyerera iye wobvala cokometsetsa, nimukati naye, Inu mukhale apa pabwino; ndipo mukati kwa wosaukayo, Iwe, ima uko, kapena, khala pansi pa mpando wa mapazi anga;

4 kodi simunasiyanitsa mwa inu nokha, ndi kukhala oweruza oganizira zoipa?

5 Mverani, abale anga okondedwa; kodi Mulungu sanasankha osauka a dziko lapansi akhale olemera ndi cikhulupiriro, ndi olowa nyumba a ufumu umene adaulonieza kwa iwo akumkonda iye?

6 Koma inu mumanyoza munthu wosauka. Kodi sakusautsani inu acuma, nakukokerani iwowa ku mabwalo a mirandu?

7 Kodi sacitira mwano iwowa dzina lokomali muitanidwa nalo?

8 Koma ngati mucita cikwanirire lamulolo lacifumu, monga mwa malembo, Uzikonda mnzako monga udzikonda wekha, mucita bwino:

9 koma ngati musamala maonekedwe, mucita ucimo, ndipo mutsutsidwa ndi cilamulo monga olakwa.

10 Pakuti amene ali yense angasunge malamulo onse, koma akakhumudwa pa limodzi, iyeyu wacimwira onse.

11 Pakuti Iye wakuti, Usacite cigololo, anatinso, Usaphe. Ndipo ukapanda kucita cigololo, koma ukapha, wakhala wolakwira lamulo.

12 Lankhulani motero, ndipo citani motero, monga anthu amene adzaweruzidwa ndi lamulo la ufulu.

13 Pakuti ciweruziro ciribe cifundo kwa iye amene sanacita cifundo; cifundo cidzitamandira kutsutsana naco ciweruziro.

14 Cipindulocace nciani, abale anga, munthu akanena, Ndiri naco cikhulupiriro, koma alibe nchito? Kodi cikhulupiriroco cikhoza kumpulumutsa?

15 Mbale kapena mlongo akakbalawausiwa, nieikamsowa cakudya ca tsiku lace,

16 ndipo wina wa inu akanena nao, Mukani ndi mtendere, muitapfunde ndi kukhuta; osawapatsa iwo zosowa za pathupi; kupindula kwace nciani?

17 Momwemonso cikhulupiriro, cikapanda kukhala nazo nchito, cikhala cakufa m'kati mwacemo.

18 Koma wina akati, Iwe uli naco cikhulupiriro, ndipo ine ndiri nazo nchito; undionetse ine cikhulupiriro cako copanda nchito zako, ndipo ine ndidzakuonetsa iweeikhulupiriro canga coturuka m'nchito zanga.

19 Ukhulupirira iwe kuti Mulungu ali mmodzi; ucita bwino; ziwanda zikhulupiranso, ndipo zinthunthumira.

20 Koma ufuna kuzindikira kodi, munthu wopanda pace iwe, kuti cikhulupiriro copanda nchito ciri cabe?

21 Abrabamu kholo lathu, sanayesedwa wolungama ndi nchito kodi, paja adapereka mwana wace Isake nsembe pa guwa la nsembe?

22 Upenya kuti cikhulupiriro cidacita pamodzi ndi nchito zace, ndipo moturuka mwa nchito cikhulupiriro cidayesedwa cangwiro;

23 ndipo anakwaniridwa malembo onenawa, Ndipo Abrahamu anakhulupirira Mulungu, ndipo kudawerengedwa kwa iye cilungamo; ndipo anachedwa bwenzi la Mulungu.

24 Mupenya kuti munthu ayesedwa wolungama ndi nchito yace, osati ndi cikhulupiriro cokha.

25 Ndipo momwemonso sanayesedwa wolungama Rahabi mkazi wa damayo ndi nchito kodi, popeza adalandira amithenga, nawaturutsa adzere njira yina?

26 Pakuti monga thupi lopanda mzimu liri lakufa, koteronso cikhulupiriro copanda nchito ciri cakufa.

3

1 Musakhale aphunzitsi ambiri, abale anga, podziwa kuti tidzalangika koposa.

2 Pakuti timakhumudwa tonse pa zinthu zambiri. Munthu akapanda kukhumudwa pa mau, iye ndiye munthu wangwiro, wokhoza kumanganso thupi lonse.

3 Koma ngati tiikiraakavalo zogwirira m'kamwa mwao atimvere, tipotolozanso thupi lao Ionse,

4 Taonani, zombonso, zingakhale zazikuru zotere, nizitengedwa ndi mphepo zolimba, zipotozeka ndi tsigiro laling'ono ndithu kumene kuli konse afuna wogwira tsigiro.

5 Kotero lilimenso liri ciwalo cacing'ono, ndipo lidzikuzira zazikuru, Taonani, kamoto kakang'ono kayatsa nkhuni zambiri!

6 Ndipo lilime ndilo moto; ngati dziko la cosalungama mwa ziwalo zathu laikika lilime, ndili lodetsa thupi lonse, niliyatsa mayendedwe a cibadwidwe, ndipo liyatsidwa ndi gehena.

7 Pakuti mtundu uli wonse wa nyama ndi wa mbalamenso, wa zokwawa, ndi wa zam'nyanja, zimazoloweretsedwa, ndipo zazoloweretsedwa ndi anthu;

8 koma lilime palibe munthu akhoza kulizoloweretsa; liri coipa cotakataka, lodzala ndi ululu wakupha.

9 Timayamika Ambuye ndi Atate nalo; nalonso timatemberera anthu, okhala monga mwa mafanizidwe a Mulungu;

10 mocokera m'kamwa momwemo muturuka ciyamiko ndi temberero. Abale anga, izi siziyenera kutero.

11 Kodi kasupe aturutsira pa una womwewo madzi okoma ndi owawa?

12 Kodi mkuyu ukhoza kubala azitona, abale anga, kapena mpesa kubala nkhuyu? Kotero madzi amcere sakhoza kuturutsa okoma.

13 Ndani ali wanzeru, ndi waluso mwa inu? Aonetsere ndi mayendedwe ace abwino nchito zace mu nzeru yofatsa.

14 Koma mukakhala nako kaduka kowawa, ndi cotetana m'mtima mwanu, musadzitamandira, ndipo musamanama potsutsana naco coonadi.

15 Nzeru iyi, sindiyo yotsika kumwamba, komatu iri ya padziko, ya cifuniro ca cibadwidwe, ya ziwanda.

16 Pakuti pomwe pali kaduka ndi zotetana, pamenepo pali cisokonekero ndi cocita coipa ciri conse.

17 Koma nzeru yocokera kumwamba iyamba kukhala yoyera, nikhalanso yamtendere, yaulere, yomvera bwino, yodzala cifundo ndi zipatso zabwino, yopanda tsankhu, yosadzikometsera pamaso.

18 Ndipo cipatso ca cilungamo cifesedwa mumtendere kwa iwo akucita mtendere.

4

1 Zicokera kuti nkhondo, zicokera kuti zolimbana mwa inu? Kodi sizicokera ku zikhumbitso zanu zocita nkhondo m'ziwalo zanu?

2 Mulakalaka, ndipo zikusowani; mukupha, nimucita kaduka, ndipo simukhoza kupeza; mulimbana, nimucita nkhondo; mulibe kanthu, cifukwa simupempha.

3 Mupempha, ndipo simulandira, popeza mupempha koipa, kuti mukacimwaze pocita zikhumbitso zanu.

4 Akazi acigololo inu, kodi simudziwa kuti ubwenzi wa dziko lapansi uti udani ndi Mulungu? Potero, iye amene afuna kukhala bwenzi la dziko lapansi adziika mdani wa Mulungu.

5 Kodi muyesa kapena kuti malembo angonena cabe? Kodi Mzimuyo adamkhalitsa mwa ife akhumbitsa kucita nsanje?

6 Koma apatsa cisomo coposa. Potero anena malembo, Mulungu akaniza odzikuza, koma apatsa cisomo odzicepetsa.

7 Potero mverani Mulungu; koma kanizani mdierekezi, ndipo adzakuthawani inu.

8 Yandikirani kwa Mulungu, ndipo adzayandikira kwa inu, Sambani m'manja, ocimwa inu; yeretsani mitima, a mitima iwiri inu.

9 Khalani osautsidwa, lirani, lirani misozi; kuseka kwanu kusanduke kulira, ndi cimwemwe canu cisanduke cisoni.

10 Dzicepetseni pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani.

11 Musamanenerana, abale. Wonenera mbale, kapena woweruza mbale wace, anenera lamulo, naweruza lamulo: koma ngati uweruza lamulo, suliwocita lamulo, komatu woweruza.

12 Woika lamulo ndi woweruza ndiye mmodzi, ndiye amene akhoza kupulumutsa ndi kuononga; koma iwe woweruza mnzako ndiwe yani?

13 Nanga tsono, inu akunena, Lero kapena mawa tidzapita kulowa ku mudzi wakuti wakuti, ndipo tidzagonerako ndi kutsatsa malonda, Ddi kupindula nao;

14 inu amene simudziwa cimene cidzagwa mawa. Moyo wanu uli wotani? Pakuti muli utsi, wakuonekera kanthawi, ndi pamenepo ukanganuka.

15 Mukadanena inu, Akalola Mulungu, ndipo tikakhala ndi moyo, tidzacita kakuti kakuti.

16 Koma tsopano mudzitamandira m'kudzikuza kwanu; kudzitamandira kuli konse kotero nkoipa.

17 Potero kwa iye amene adziwa kucita bwino, ndipo sacita, kwa iye kuli cimo.

5

1 Nanga tsono acuma inu, lirani ndi kucema cifukwa ca masautso anu akudza pa inu,

2 Cuma canu caola ndi zobvala zanu zajiwa ndi njenjete.

3 Golidi wanu ndi siliva wanu zacita dzimbiri, ndipo dzimbiri lace lidzacita mboni zoneneza Inu ndipo zidzadya nyama yanu ngat: moto. Mwadzikundikira cuma masiku otsiriza.

4 Taonani, mphotho ya anchitowo anasenga m'minda yanu, yosungidwa ndi inu powanyenga, ipfuula; ndipo mapfuulc a osengawo adalowa m'makutu a Ambuye wa makamu.

5 Mwadyerera padziko, ndipo mwacita zokukondweretsani; mwadyetsa mitima yanu m'tsiku lakupha.

6 Munamtsutsa, munapha wolungamayo, iye sakanizainu.

7 Potero, lezani mtima, abale, kufikira kudza kwace kwa Ambuye. Taonani, wolima munda alindira cipatso cofunikatu ca dziko, ndi kuleza mtima naco kufikira cikalandira mvula ya myundo ndi masika,

8 Lezani mtima inunso, limbitsani mitima yanu; pakuti kudza kwace kwa Ambuye kuyandikira.

9 Musaipidwe wina ndi mnzace, abale, kuti mungaweruzidwe. Taonani, woweruza aima pakhomo.

10 Tengani, abale, citsanzo ca kumva zowawa ndi kuleza mtima, aneneri ameneanalankhulam'dzina la Ambuyeo

11 Taonani tiwayesera odala opirirawo; mudamva za cipiriro ca Yobu, ndipo mwaona citsiriziro ca Ambuye, kuti Ambuye ali wodzala cikondi, ndi wacifundo.

12 Koma makamaka, abale anga, musalumbire, kungakhale kuchula mwamba kapena dziko, kapena lumbiro lina liri lonse; koma inde wanu akhale inde, ndi iai wanu akha; le iai; kuti mungagwe m'ciweruziro.

13 Kodi wina wa inu akumva zowawa? Apemphere, Kodi wina asekera? Ayimbire.

14 Pali wina kodi adwala mwa inu? Adziitanire akuru a Mpingo, ndipo apemphere pa iye, atamdzoza ndi mafuta m'dzina la Ambuye:

15 ndipo pemphero la cikhulupiriro lidzapulumutsa wodwalayo, ndipo Ambuye adzamuukitsa; ndipo ngati adacita macimo adzakhululukidwa kwa iye.

16 Cifukwa cace mubvomerezane wina ndi mnzace macimo anu, ndipo mupempherere wina kwa mnzace kuti muciritsidwe. Pemphero la munthu wolungama likhoza kwakukuru m'macitidweace.

17 Eliya anali munthu wakumva zomwezi tizimva ife, ndipo anapemphera cipempherere kuti isabvumbe mvula; ndipo, siinagwa mvula pa dzikozaka zitatu kudza miyezi isanu ndi umodzi.

18 Ndipo anapempheranso; ndipo m'mwamba munatsika mvula, ndi dziko lidabala zipatso zace.

19 Abale anga, ngati wina wa inu asocera posiyana ndi coonadi, ndipo ambweza iye mnzace;

20 azindikire, kuti iyeamene abweza wocimwa ku njira yace yosocera adzapulumutsa munthu kwa imfa, ndipo adzabvundikira macimo aunyinji.