1 MAU a Amosi, amene anali mwa oweta ng'ombe a ku Tekoa, ndiwo amene anawaona za Israyeli masiku a Uziya mfumu ya Yuda, ndi masiku a Yerobiamu mwana wa Yoasi mfumu ya Israyeli, zitatsala zaka ziwiri cisanafike cibvomezi.
2 Ndipo anati, Yehova adzadzuma ali m'Ziyoni, nadzamveketsa mau ace ali m'Yerusalemu; podyetsa abusa padzacita cisoni, ndi mutu wa Karimeli udzauma.
3 Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Damasiko, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anapuntha Gileadi ndi zopunthira zacitsulo;
4 koma ndidzatumiza moto ku nyumba ya Hazaeli, ndipo udzanyeketsa nyumba zacifumu za Benihadadi.
5 Ndipo ndidzatyola mpiringidzo wa Damasiko, ndi kulikha okhala m'cigwa ca Aveni, ndi iye wogwira ndodo yacifumu m'Betedeni; ndi anthu a Aramu adzalowa ndende ku Kiri, ati Yehova.
6 Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Gaza, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anatenga ndende anthu onse kuwapereka kwa Edomu;
7 koma ndidzatumiza moto pa linga la Gaza, ndipo udzatha nyumba zace zacifumu;
8 ndipo ndidzalikha okhala m'Asidodi, ndi iye wogwira ndodo yacifumu m'Asikeloni; ndipo ndidzabwezera Ekroni dzanja langa limlange; ndi Afilisti otsala adzatayika, ati Ambuye Yehova.
9 Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Turo, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anapereka anthu onse kwa Edomu, osakumbukila pangano lacibale;
10 koma ndidzatumiza moto pa linga la Turo, ndipo udzanyeketsa nyumba zace zacifumu.
11 Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Edomu, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza analondola mphwace ndi lupanga, nafetsa cifundo cace conse, ndi mkwiyo wace unang'amba cing'ambire, nasunga mkwiyo wace cisungire;
12 koma ndidzatumiza moto pa Temani, udzanyeketsa nyumba zacifumu za Bozira.
13 Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za ana a Amoni, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anatumbula akazi ali m'pakati a Gileadi, kuti akuze malire ao;
14 koma ndidzayatsa moto pa linga la Raba, udzanyeketsa nyumba zacifumu zace, ndi kupfuula tsiku la nkhondo, ndi namondwe, tsiku la kabvumvulu;
15 ndipo mfumu yao idzalowa kundende, iyo ndi akalonga ace pamodzi, ati Yehova.
1 Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Moabu, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anatentha mafupa a mfumu ya ku Edomu asanduke njereza;
2 koma ndidzatumiza moto pa Moabu, udzanyeketsa nyumba zacifumu za Kerioti; ndipo Moabu adzafa ndi phokoso, ndi kupfuula, ndi mau a lipenga;
3 ndipo ndidzalikha woweruza pakati pace, ndi kupha akalonga ace onse, ati Yehova.
4 Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Yuda, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza akaniza cilamulo ca Yehova, osasunga malemba ace; ndipo awalakwitsa mabodza ao amene makolo ao anawatsata;
5 koma ndidzatumiza moto pa Yuda, udzanyeketsa nyumba zacifumu za m'Yerusalemu.
6 Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Israyeli, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza agulitsa wolungama ndi ndalama, ndi wosowa cifukwa ca nsapato;
7 ndiwo amene aliralira pfumbi lapansi liri pamutu pa wosauka, napotoza njira ya wofatsa; ndipo munthu ndi atate wace amuka kwa namwali yemweyo, kuti aipse dzina langa loyera;
8 nagona pansi pa zopfunda za cikole ku maguwa a nsembe ali onse, ndi m'nyumba ya Mulungu wao akumwa vinyo wa iwo olipitsidwa.
9 Koma ndinaononga Ine pamaso pa Aamori, amene msinkhu wao unanga msinkhu wa mikungudza, nakhala nayo mphamvu ngati thundu; koma ndinaononga zipatso zao m'mwamba, ndi mizu yao pansi.
10 Ndipo ndinakukwezani kucokera m'dziko la Aigupto, ndi kukutsogolerani zaka makumi anai m'cipululu, kuti mulandire dziko la Aamori likhale colowa canu.
11 Ndipo ndinaukitsa mwa ana anu aneneri, ndi mwa anyamata anu Anaziri. Si momwemo, inu ana a Israyeli, ati Yehova?
12 Koma munamwetsa Anaziri vinyo, ndi kulamulira aneneri ndi kuti, Musamanenera.
13 Taonani, ndidzakupsinjani m'malo mwanu, monga lipsinja gareta lodzala ndi mitolo fwa.
14 Ndipo populumukirapo padzasowera waliwiro, ndi wamphamvu; sadzalimbikitsa mphamvu yace, ndi ngwazi siidzapulumutsa moyo wace;
15 ndi wokoka uta sadzalimbika, ndi waliwiro sadzadzipulumutsa; ngakhale woyenda pa akavalo sadzapulumutsa moyo wace;
16 ndi wolimba mtima mwa ngwazi adzathawa wamarisece tsiku lomwelo, ati Yehova.
1 Tamverani mau awa akunenerani Yehova motsutsa, inu ana a Israyeli, kulinenera banja lonse ndinalikweza kuliturutsa m'dziko la Aigupto, ndi kuti,
2 Inu nokha ndinakudziwani mwa mabanja onse a pa dziko lapansi, m'mwemo ndidzakulangani cifukwa ca mphulupulu zanu zonse.
3 Kodi awiri adzayenda pamodzi asanapanganiranetu?
4 Kodi mkango udzabangula m'nkhalango wosakhala nayo nyama? Kodi msona wa mkango udzalira m'ngaka mwace usanagwire kanthu?
5 Kodi mbalame idzakodwa mumsampha pansi popanda msampha woichera? Kodi msampha ufamphuka pansi wosakola kanthu?
6 Kodi adzaomba lipenga m'mudzi osanieniemera anthu? Kodi coipa cidzagwera mudzi osacicita Yehova?
7 Pakuti Ambuye Yehova sadzacita kanthu osaulula cinsinsi cace kwa atumiki ace aneneri.
8 Mkango ukabangula, ndani amene saopa? Ambuye Yehova wanena, ndani amene sanenera?
9 Bukitsani ku nyumba zacifumu za Asidodi, ndi ku nyumba zacifumu za m'dziko la Aigupto, nimuziti, Sonkhanani pa mapiri a Samariya, ndipo penyani masokosero akuru m'menemo, ndi ozunzika m'kati mwace.
10 Pakuti sadziwa kucita zolungama, amene akundika zaciwawa ndi umbala m'nyumba zao zacifumu, ati Yehova.
11 Cifukwa cace, atero Ambuye Yehova, Padzakhala mdani pozungulira pace pa dziko, nadzatsitsa kukucotsera mphamvu yako; ndi za m'nyumba zako zacifumu adzazifunkha.
12 Atero Yehova, Monga mbusa alanditsa m'kamwa mwa mkango miyendo iwiri, kapena kansonga ka khutu, momwemo adzalanditsidwa ana a Israyeli okhala pansi m'Samariya, m'ngondya ya guwa logonapo, ndi pa mitsamiro ya kama.
13 Tamverani inu, mucitire umboni wotsutsa nyumba ya Yakobo, ati Ambuye Yehova Mulungu wa makamu.
14 Pakuti tsiku lakumlanga Israyeli cifukwa ca zolakwa zace, ndidzalanganso maguwa a nsembe a ku Beteli; ndi nyanga za guwa la nsembe zidzadulidwa, nizidzagwa pansi.
15 Ndipo ndidzakantha nyumba ya nyengo yacisanu, pamodzi ndi nyumba ya nyengo yadzuwa; ndi nyumba zaminyanga zidzaonongeka; ndi nyumba zazikuruzo zidzatha, ati Yehova.
1 Tamverani mau awa, inu ng'ombe zazikazi za ku Basana, zokhala m'phiri la Samariya, zosautsa aumphawi, zopsinja osowa, zonena kwa ambuyao, Bwerani naco, timwe.
2 Ambuye Yehova walumbira pali ciyero cace, kuti taonani, adzakugwerani masiku akuti adzakucotsani ndi zokowera, ndi otsala anu ndi mbedza.
3 Ndipo mudzaturukira popasuka linga, yense m'tsogolo mwace, ndi kutayika ku Harimoni, ati Yehova.
4 Idzani ku Beteli, mudzalakwe ku Giligala, nimucurukitse zolakwa, nimubwere nazo nsembe zanu zophera m'mawa ndi m'mawa, magawo anu akhumi atapita masiku atatu atatu;
5 nimutenthe nsembe zolemekeza zacotupitsa, nimulalikire nsembe zaufulu, ndi kuzimveketsa; pakuti ici mucikonda, inu ana a Israyeli, ati Ambuye Yehova.
6 Ndipo ine ndakupatsaninso mano oyera m'midzi yanu yonse, ndi kusowa mkate m'malo mwanu monse; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.
7 Ndipo Ine ndakumanani mvula, itatsala miyezi itatu isanafika nyengo yakukolola; ndipo ndinabvumbistira mudzi umodzi mvula, osabvumbitsira mudzi wina; munda wina unabvumbidwa mvula, ndi m'munda mosabvumbidwa mvula munafota.
8 M'mwemo midzi iwiri kapena itatu inayenda peyupeyu ku mudzi umodzi kukamwa madzi, koma sanakhuta; koma simunai bwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.
9 Ndinakukanthani ndi cinsikwi ndi cinoni; minda yanu yocuruka yamipesa, ndi yamikuyu, ndi yaazitona, yaonongeka ndi cirimamine; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.
10 Ndinatumiza mliri pakati panu monga m'Aigupto; anyamata anu ndawapha ndi lupanga, ndi kutenga akavalo anu; ndipo ndinakweretsa kununkha kwa cigono canu kufikitsa kumphuno kwanu; ikoma simunabwerera kudzakwa Ine, ati Yehova.
11 Ndinagubuduza ena mwa inu, monga umo Mulungu anagubuduzira Sodomu ndi Gomora; ndipo inu munali ngati muuni wofumulidwa kumoto; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.
12 Cifukwa cace ndidzatero nawe, Israyeli; popeza ndidzakucitira ici, dzikonzeretu kukomana ndi Mulungu wako, Israyeli.
13 Pakuti taona, Iye amene aumba mapiri, nalenga mphepo, nafotokozera munthu maganizo ace, nasanduliza m'mawa ukhale mdima, naponda pa misanje ya dziko lapansi, dzina lace ndiye Yehova Mulungu wamakamu.
1 Tamverani mau awa ndinenawa, akhalire inu nyimbo ya maliro, nyumba ya Israyeli inu.
2 Namwali wa Israyeli wagwa, sadzaukanso; wagwetsedwa pa nthaka yace, palibe womuutsa.
3 Pakuti atero Ambuye Yehova, M'nyumba ya Israyeli, mudzi woturukamo cikwi cimodzi adzautsalira zana limodzi, ndi uwu woturukamo zana limodzi adzautsalira khumi.
4 Pakuti atero Yehova kwa nyumba ya Israyeli, Mundifunefune Ine, ndipo mudzakhala ndi moyo;
5 koma musamafuna Beteli, kapena kumalowa m'Giligala; musamapita ku Beereseba; pakuti Giligala adzalowadi m'ndende, ndi Beteli adzasanduka cabe.
6 Funani Yehova, ndipo mudzakhala ndi mayo; angabuke ngati moto m'nyumba ya Yosefe, ndipo unganyeke wopanda wakuzima m'Beteli;
7 inu osintha ciweruzo cikhale civumulo, nimugwetsa pansi cilungamo,
8 Iye wakulenga Nsangwe ndi Akamwiniatsatana, nasanduliza mdima wandiweyani ukhale m'mawa, nasanduliza usana ude ngati usiku, wakuitana madzi a m'nyanja, nawatsanulira pa dziko lapansi, dzina lace ndiye Yehova;
9 wakufikitsa cionongeko pa wamphamvu modzidzimuka, cionongeko nicigwera linga,
10 Iwo adana naye wodzudzula kucipata, nanyansidwa naye wolunjikitsa mau.
11 Popeza tsono mupondereza aumphawi, ndi kumsonkhetsa tirigu; mwamanga nyumba za miyala yosema, koma simudzakhala m'mwemo; mwaoka minda ya mipesa yokonda, koma simudzamwa vinyo wace.
12 Pakuti ndidziwa kuti zolakwa zanu nzocuruka, ndi macimo anu ndi olimba, inu akusautsa olungama, akulandira cokometsera mlandu, akukankha osowa kucipata.
13 Cifukwa cace wocenierayo akhala cete nthawi yomweyo; pakuti ndiyo nthawi yoipa.
14 Funani cokoma, si coipa ai; kuti mukhale ndi moyo; motero Yehova Mulungu wamakamu adzakhala ndi inu, monga munena.
15 Danani naco coipa, nimukonde cokoma; nimukhazikitse ciweruzo kucipata; kapena Yehova Mulungu wa makamu adzacitira cifundo otsala a Yosefe.
16 Cifukwa cace atero Yehova, Mulungu wa makamu, Ambuye, M'makwalala onse mudzakhala kulira, ndi m'miseu yonse adzati, Kalanga ine! kalanga ine! nadzaitana wakumunda adze kumaliro, ndi odziwa maliridwe a nthetemya alire.
17 Ndi m'minda yonse yamipesa mudzakhala kulira, pakuti ndipita pakati pako, ati Yehova.
18 Tsoka inu akufuna tsiku la Yehova! mudzapindulanji nalo tsiku la Yehova? ndilo mdima, si kuunika ai.
19 Kudzakhala monga munthu akathawa mkango, ndi cimbalangondo cikomana naye; kapena akalowa m'nyumba, natsamira kukhoma ndi dzanja lace, nimluma njoka.
20 Kodi tsiku la Yehova silidzakhala la mdima, si la kuunika ai? lakuda bii, lopanda kuwala m'menemo?
21 Ndidana nao, ndinyoza madyerero anu, sindidzakondwera nao masonkhano anu oletsa.
22 Inde, mungakhale mupereka kwa Ine nsembe zanu zopsereza, ndi nsembe zaufa, sindidzazilandira Ine; ndinsembe zoyamika za ng'ombe zanu zonenepa, sindidzazisamalira Ine.
23 Mundicotsere phokoso la nyimbo zanu; sindifuna kumva mayimbidwe a zisakasa zanu.
24 Koma ciweruzo ciyende ngati madzi, ndi cilungamo ngati mtsinje wosefuka.
25 Ngati munabwera nazo kwa Ine nsembe zophera ndi zaufa zaka makumi anai m'cipululu, inu nyumba ya Israyeli?
26 Inde mwasenza hema wa mfumu yanu, ndi tsinde la mafano anu, nyenyezi ya mlungu wanu, amene mudadzipangira.
27 M'mwemo ndidzakutengani kumka nanu kundende kutsogolo kwa Damasiko, ati Yehova, amene dzina lace ndiye Mulungu wa makamu.
1 Tsoka osalabadirawo m'Ziyoni, ndi iwo okhazikika m'phiri la Samariya, ndiwo anthu omveka amtundu woposa wa anthu, amene nyumba ya Israyeli iwafikira!
2 Pitani ku Kaline, nimuone; kucokera komweko mupite ku Hamati wamkulu mutsikire ku Gati wa Afilisti; kodi awo ndi okoma koposa maufumu ano? kapena malire ao aposa malire anu?
3 Inu akutalikitsa tsiku loipa, ndi kusendeza pafupi mpando waciwawa;
4 ogona pa makama aminyanga, nadzithinula pa maguwa ao ogonapo, nadya ana a nkhosa a ku zoweta, ndi ana a ng'ombe ocoka pakati pa khola;
5 akungoyimba kutsata maliridwe a zeze, nadzilingiririra zoyimbira nazo Ingati Davide;
6 akumwera vinyo m'zipanda, nadzidzoza ndi mafuta abwino oposa, osagwidwa cisoni ndi kutyoka kwa Yosefe.
7 Cifukwa cace tsono, adzatengedwa ndende ndi oyamba kutengedwa ndende; ndi phokoso la iwo odzithinula lidzapita.
8 Ambuye Yehova walumbira pali Iye mwini, ati Yehova Mulungu wa makamu, Ndinyansidwa nako kudzikuza kwa Yakobo, ndidana nazo nyumba zace zacifumu; m'mwemo ndidzapereka mudzi, ndi zonse ziri m'menemo.
9 Ndipo kudzacitika, mukatsala amuna khumi m'nyumba imodzi, adzafa.
10 Ndipo mbalewace wa munthu akamnyamula, ndiye womtentha, kuturutsa mafupa m'nyumba, nakati kwa iye ali m'kati mwa nyumbamo, Atsala wina nawe kodi? nakati, lai; pamenepo adzati, Khala cete; pakuti sitingachule dzina la Yehova.
11 Pakuti taonani, Yehova walamulira, nadzakantha nyumba yaikuru icite mpata, ndi nyumba yaing'ono icite mindala.
12 Kodi akavalo adzathamanga pathanthwe? kodi adzalimako ndi ng'ombe? pakuti mwasanduliza ciweruzo cikhale ndulu, ndi cipatso ca cilungamo cikhale civumulo;
13 inu okondwera naco copanda pace, ndi kuti, Kodi sitinadzilimbitsa tokha mwa mphamvu yathu yathu?
14 Pakuti taonani, ndidzakuutsirani mtundu wa anthu, nyumba ya Israyeli, ati Yehova Mulungu wa makamu; ndipo adzakupsinjani kuyambira polowera ku Hamati kufikira mtsinje wa kucidikha.
1 Ambuye Yehova anandionetsa cotere; ndipo taonani, anaumba dzombe, poyamba kuphuka kwa maudzu a cibwereza; ndipo taonani, ndico cibwereza atawasengera mfumu.
2 Ndipo kunacitika m'mene lidatha kudya msipu wa dziko, ndinati, Ambuye Yehova, khululukiranitu Yakobo; adzakhala ciriri bwanji? popeza ndiye wamng'ono.
3 Ndipo Yehova anacileka. Sicidzacitika, ati Yehova.
4 Ambuye Yehova anandionetsa cotere; ndipo taonani, Ambuye Yehova anaitana kuti atsutse ndi moto; ndipo unanyambita cakudya cacikuru ukadanyambitanso dziko.
5 Pamenepo ndinati, Ambuye Yehova, Iekanitu; Yakobo adzakhala ciriri bwanji? pakuti ali wamng'ono.
6 Ndipo Yehova anacileka. Ici comwe sicidiacitika, ati Ambuye Yehova.
7 Anandionetsa cotere; ndipo taonani, Ambuye anaima pa khoma lomangiwda ndi cingwe colungamitsira ciriri; ndi cingwe colungamitsira ciriri m'dzanja lace.
8 Ndipo Yehova anati kwa ine, Amosi, uona ciani? Ndipo ndinati, Cingwe colungamitsira ciriri. Nati Ambuye, Taona, ndidzaika cingwe colungamitsira ciriri pakati pa anthu anga Israyeli, sindidzawalekanso:
9 ndi misanje ya Isake idzakhala bwinja; ndi malo opatulika a Israyeli adzapasuka; ndipo ndidzaukira nyumba ya Yerobiamu ndi lupanga.
10 Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza kwa Yerobiamu mfumu ya Israyeli, ndi kuti, Amosi wapangira inu ciwembu pakati pa nyumba ya Israyeli; dziko silikhoza kulola mau ace onse.
11 Pakuti atero Amosi, Yerobiamu adzafa ndi lupanga, ndi Israyeli adzatengedwadi ndende, kucoka m'dziko lace.
12 Amaziya anatinso kwa Amosi, Mlauli iwe, coka, thawira ku dziko la Yuda, nudye, nunenere komweko;
13 koma usaneneranso ku Beteli; pakuti pamenepo mpa malo opatulika a mfumu, ndiyo nyumba yacifumu.
14 Pamenepo Amosi anayankha, nati kwa Amaziya, Sindinali mneneri, kapena mwana wa mneneri, koma ndinali woweta ng'ombe, ndi wakuchera nkhuyu;
15 ndipo Yehova ananditenga ndirikutsata nkhosa, nati kwa ine Yehova, Muka, nenera kwa anthu anga Israyeli.
16 Cifukwa cace tsono, tamvera mau a Yehova, Iwe ukuti, Usamanenera cotsutsana ndi Israyeli, usadonthetsa mau akutsutsana ndi nyumba ya Isake;
17 cifukwa cace atero Yehova, Mkazi wako adzakhala wadama m'mudzi, ndi ana ako amuna ndi akazi adzagwa ndi lupanga, ndi dziko lako lidzagawanidwa ndi kuyesa cingwe, ndi iwe mwini udzafa m'dziko lodetsedwa; ndipo Israyeli adzatengedwadi ndende kucoka m'dziko lace.
1 Ambuye Yehova anandionetsa cotere; ndipo taonani, mtanga wa zipatso zamalimwe.
2 Ndipo anati, Amosi uona ciani? Ndipo ndinati, Mtanga wa zipatso zamalimwe. Nati Yehova kwa ine, Citsiriziro cafikira anthu anga Israyeli, sindidzawalekanso.
3 Koma nyimbo za kukacisi zidzasanduka kubuma tsiku ilo, ati Ambuye Yehova; mitembo idzacuruka; adzaitaya pali ponse padzakhala zii.
4 Tamverani ici, inu akumeza aumphawi, ndi kuwatha ofatsa m'dziko, ndi kuti,
5 Mwezi wokhala upita liti, kuti tigulitse dzinthu? ndi Sabata, kuti titsegulire tirigu? ndi kucepsa efa, ndi kukuliitsa sekeli, ndi kucenjerera nayo miyeso yonyenga;
6 kuti tigule osauka ndi ndarama, ndi aumphawi ndi nsapato, ndi kugulitsa nsadwa za tirigu.
7 Yehova walumbira pali kudzikuza kwa Yakobo, Ngati ndidzaiwala konse nchito zao ziri zonse?
8 Kodi dziko silidzanjenjemera cifukwa ca ici, ndi kulira ali yense wokhalamo? inde lidzakwera lonseli ngati madzi a m'mtsinje; lidzagwedezeka, ndi kutsikanso ngati mtsinje wa Aigupto,
9 Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo, ati Ambuye Yehova, ndidzalowetsa dzuwa usana, ndi kudetsa dziko pausana poyera.
10 Ndipo ndidzasanduliza madyerero anu, akhale maliro, ndi nyimbo zanu zikhale za maliro, ndi kufikitsa ziguduli m'cuuno monse, ndi mpala pa mutu uli wonse; nadzakhala ngati maliro a mwana mmodzi yekha, ndi citsiriziro cace ngati tsiku lowawa.
11 Taonani, akudza masiku, ati Ambuye Yehova, akuti ndidzatumiza njala m'dzikomo, si njala ya mkate kapena ludzu la madzi, koma njala ya kumva mau a Yehova.
12 Ndipo adzayendayenda peyupeyu kuyambira kunyanja kufikira kunyanja ndi kuyambira kumpoto kufikira kum'mawa; adzathamangathamanga kufunafuna mau a Yehova, koma osawapeza.
13 Tsiku lomwelo anamwali okongola ndi anyamata adzakomoka nalo ludzu.
14 Iwo akulumbira ndi kuchula cimo la Samariya, ndi kuti, Pali Mulungu wako, Dani; ndipo, Pali moyo wa njira ya ku Beereseba, iwowa adzagwa, osaukanso konse.
1 Ndinaona Ambuye alikuima pa guwa la nsembe, nati Iye, Kantha mitu ya nsanamira, kuti ziundo zigwedezeke; nuphwanye mitu yao yonse; ndipo ndidzapha otsiriza ao ndi lupanga; wothawayo mwa iwo sadzathawadi, ndi wopulumukayo mwaiwosadzapulumukadi.
2 Angakhale akumba mpaka kunsi kwa manda, dzanja langa lidzawatenga kumeneko; angakhale akwera kumwamba, ndidzawatsitsa komweko.
3 Angakhale abisala pamwamba pa Karimeli, ndidzawapwaira ndi kuwatenga komweko; angakhale abisala pamaso panga pansi pa nyanja, kumeneko ndidzalamulira njoka, ndipo idzawaluma.
4 Angakhale alowa ndende pamaso pa adani ao, kumeneko ndidzalamulira lupanga, ndipo lidzawapha; ndipo ndidzayang'anitsa maso anga kwa iwowa, kuwacitira coipa, si cokoma ai.
5 Pakuti Ambuye Yehova wa makamu ndiye amene akhudza dziko, nilisungunuka; ndi onse okhalamo adzacita maliro; ndipo lidzakwera lonseli ngati madzi a m'nyanja; nilidzatsikanso ngati nyanja ya m'Aigupto;
6 ndiye amene amanga zipinda zace zosanja m'mwamba, nakhazika tsindwi lace pa dziko lapansi; Iye amene aitana madzi a m'nyanja, nawatsanulira padziko; dzina lace ndiye Yehova.
7 Kodi simukhala kwa Ine ngati ana a Kusi, inu ana a Israyeli? ati Yehova. Sindinakweza Israyeli ndine, kumturutsa m'dziko la Aigupto, ndi Afilisti ku Kafitori, ndi Aaramu ku Kiri?
8 Taonani, maso a Ambuye Yehova ali pa ufumu wocimwawo, ndipo ndidzauononga kuucotsa pa dziko lapansi; pokhapo sindidzaononga nyumba ya Yakobo kuitha konse, ati Yehova.
9 Pakuti taonani, ndidzalamulira, ndipo ndidzapeta nyumba ya Israyeli mwa amitundu onse, monga apeta tirigu m'licero; koma silidzagwa pansi diso, ndi limodzi lonse.
10 Ocimwa onse a anthu anga adzafa ndi lupanga, ndiwo amene akuti, Coipa sicidzatipeza, kapena kutidulira.
11 Tsiku lomwelo ndidzautsa msasa wa Davide udagwawo, ndi kukonzanso zopasuka zace; ndipo ndidzautsa zogumuka zace, ndi kuumanga monga masiku a kalelo;
12 kuti alandire otsala a Edomu akhale colowa cao, ndi amitundu onse akuchedwa dzina langa, ati Yehova wakucita izi.
13 Taonani akudza masiku, ati Yehova, akud wolima adzapezana ndi wodula, ndi woponda mphesa adzapezana ndi wofesa, ndi mapiri adzakhetsa vinyo watsopano, ndi zitunda zonse zidzasungunuka.
14 Ndipo ndidzabwezanso undende wa anthu anga Israyeli, ndipo adzamanganso mabwinja, ndi kukhala m'menemo; nadzaoka minda ya mipesa nadzamwa vinyo wace, nadzalima minda ndi kudya zipatso zace.
15 Ndipo ndidzawaoka m'dziko mwao ndipo sadzazulidwanso m'dziko lao limene ndawapatsa, ati Yehova Mulungu wako.