1

1 KATUNDU wa mau a Yehova wa kwa Israyeli mwa Malaki.

2 Ndakukondani, ati Yehova; koma inu mukuti, Mwatikonda motani? Esau si mkulu wace wa Yakobo kodi? ati Yehova; ndipo ndinakonda Yakobo;

3 koma Esau ndinamuda, ndinasanduliza mapiri ace abwinja, ndi kupereka colowa cace kwa ankhandwe a m'cipululu.

4 Cinkana Edomu akuti, Taphwanyika, koma tidzabwera ndi kumanganso mabwinja; atero Yehova wa makamu, Adzamanga, koma Ine ndidzapasula; ndipo adzawacha, Dziko la coipa, ndiponso, Anthu amene Yehova akwiya nao cikwiyire.

5 Ndipo maso anu adzaona, nimudzati, Yehova ali wamkuru kupitirira malire a Israyeli.

6 Mwana alemekeza atate wace, ndi mnyamata mbuye wace; ngati Ine tsono ndine atate, uli kuti ulemu wanga? ngati Ine ndine mbuye, kundiopa kuli kuti? ati Yehova wa makamu kwa inu ansembe akupeputsa dzina langa. Ndipo mukuti, Tapeputsa dzina lanu motani?

7 Mupereka mkate wodetsedwa pa guwa langa la nsembe; ndipo mukuti, Takudetsani motani? M'menemo, mwakuti munena, Gome la Yehova nlonyozeka.

8 Ndipo pamene mupereka yakhungu ikhale nsembe, mukuti, Palibe coipa! ndi popereka yotsimphina ndi yodwala, palibe coipa! Kaiperekeni kwa kazembe wanu, mudzamkomera kodi? kapena adzakubvomerezani kodi? ati Yehova wa makamu.

9 Ndipo tsopano, mupepeze Mulungu, kuti aticitire cifundo; icico cicokera kwa inu; kodi Iye adzabvomereza ena a inu? ati Yehova wa makamu.

10 Mwenzi atakhala wina mwa inu wakutseka pamakomo, kuti musasonkhe moto cabe pa guwa langa la nsembe! Sindikondwera nanu, ati Yehova wa makamu, ndipo sindidzalandira capereka m'dzanja lanu.

11 Pakuti kuyambira koturukira dzuwa kufikira kolowera kwace dzina langa lidzakhala lalikuru mwa amitundu; ndipo m'malo monse adzaperekera dzina langa cofukiza ndi copereka coona; pakuti dzina langa lidzakhala lalikuru mwa amitundu, ati Yehova wa makamu.

12 Koma inu muliipsa, pakunena inu, Gome la Yehova laipsidwa, ndi zipatso zace, cakudya cace, conyozeka.

13 Mukutinso, Taonani, ncolemetsa ici! ndipo mwacipeputsa, ati Yehova wa makamu; ndipo mwabwera nazo zofunkha, ndi zotsimphina, ndi zodwala; momwemo mubwera nayo nsembe; kodi ndiyenera kuilandira ku dzanja lanu? ati Yehova.

14 Koma wotembereredwa wonyengayo, wokhala nayo yaimuna m'gulu lace, nawinda, naphera Yehova nsembe cinthu cacirema; pakuti Ine ndine mfumu yaikuru, ati Yehova wa makamu; ndipo dzina langa ndi loopsa pakati pa amitundu.

2

1 Ndipo tsono, ansembe inu, lamulo ili ndi la kwa inu.

2 Mukapanda kumvera, mukapanda kuliika mumtima mwanu, kupatsa dzina langa ulemerero, ati Yehova wa makamu, ndidzakutumizirani temberero, ndi kutemberera madalitso anu; inde, ndawatemberera kale cifukwa simuliika mumtima.

3 Taonani, ndidzaipsa mbeu cifukwa ca inu, ndi kuwaza ciphwidza pankhope panu, ndico ciphwidza ca nsembe zanu, ndipo adzakucotsani pamodzi naco.

4 Ndipo mudzadziwa kuti ndatumiza lamulo ili kwa inu, kuti cipangano canga cikhale ndi Levi, ati Yehova wa makamu.

5 Cipangano canga cinali naye ca moyo ndi ca mtendere; ndipo ndinampatsa izi kuti aope; nandiopa, naopsedwa cifukwa ca dzina langa.

6 Cilamulo ca zoona cinali m'kamwa mwace, ndi cosalungama sicinapezeka m'milomo mwace; anayenda nane mumtendere ndi moongoka, nabweza ambiri aleke mphulupulu,

7 Pakuti milomo ya wansembe iyenera kusunga cidziwitso, ndi anthu ayenera kufunafuna cilamulo pakamwa pace; pakuti iye ndiye mthenga wa Yehova wa makamu.

8 Koma inu mwapambuka m'njira; mwakhumudwitsa ambiri m'cilamulo; mwaipsa cipangano ca Levi, ati Yehova wa makamu.

9 Cifukwa cace Inenso ndakuikani onyozeka ndi ocepseka kwa anthu onse, popeza simunasunga njira zanga, koma munaweruza mwankhope pocita cilamulo.

10 Kodi sitiri naye Atate mmodzi ife tonse? sanatilenga kodi Mulungu mmodzi? Ticita monyengezana yense ndi mnzace cifukwa ninji, ndi kuipsa cipangano ca makolo athu?

11 Yuda wacha monyenga, ndi m'Israyeli ndi m'Yerusalemu mwacitika conyansa; pakuti Yuda waipsa cipatuliko ca Yehova cimene acikonda, nakwatira mwana wamkazi wa mlungu wacilendo.

12 Yehova adzalikha munthu wakucita ici, wogalamutsa ndi wobvomereza m'tnahema a Yakobo, ndi iye wopereka copereka kwa Yehova wa makamu.

13 Ndi ici mubwereza kucicita: mukuta guwa la nsembe la Yehova ndi misozi, ndi kulira, ndi kuusa moyo; momwemo Iye sasamaliranso copereka, kapena kulandira mokondwera m'dzanja lanu.

14 Koma mukuti, Cifukwa ninji? Cifukwa kuti Yehova anali mboni pakati pa iwe ndi mkazi wa ubwana wako, amene unamcitira cosakhulupirika, cinkana iye ndiye mnzako, mkazi wa pangano lako.

15 Ndipo sanatero kodi wina womtsalira mzimu? Ndipo winayo anatero bwanji? Anatero pofuna mbeu ya Mulungu. Koma sungani mzimu wanu; ndipo asamcitire monyenga mkazi wa ubwana wace ndi mmodziyense.

16 Pakuti ndidana nako kuleka kumene, ati Yehova Mulungu wa Israyeli, ndi iye wakukuta cobvala cace ndi ciwawa, ati Yehova wa makamu; cifukwa cace sungani mzimu wanu kuti musacite mosakhulupirika.

17 Mwalemetsa Yehova ndi mau anu. Koma mukuti, Tamlemetsa ndi ciani? Ndi ici cakuti munena, Yense wakucita coipa ali wokoma pamaso pa Mulungu, ndipo akondwera nao; kapena, Ali kuti Mulungu wa ciweruzo?

3

1 Taonani, ndituma mthenga wanga, kuti akonzeretu njira pamaso panga; ndipo Ambuye amene mumfuna adzadza ku Kacisi wace modzidzimutsa; ndiye mthenga wa cipangano amene mukondwera naye; taonani akudza, ati Yehova wa makamu.

2 Koma ndani adzapirira tsiku la kudza kwace? ndipo adzaima ndani pooneka Iye? pakuti adzanga moto wa woyenga, ndi sopo wa otsuka;

3 ndipo adzakhala pansi ndi kuyenga ndi kuyeretsa siliva, nadzayeretsa ana a Levi, nadzawayengetsa ngati golidi ndi siliva; pamenepo iwo adzapereka kwa Yehova zopereka m'cilungamo.

4 Pamenepo copereka ca Yuda ndi Yerusalemu cidzakomera Yehova, ngati masiku a kale lija ndi ngati zaka zoyamba zija.

5 Ndipo ndidzayandikiza kwa inu kuti ndiweruze; ndipo ndidzakhala mboni yakufulumira kutsutsa obwebweta, ndi acigololo, ndi olumbira monama; ndi iwo akunyenga wolembedwa nchito pa kulipira kwace, akazi amasiye, ndi ana amasiye, ndi wakuipsa mlandu wa mlendo, osandiopa Ine, ati Yehova wa makamu.

6 Pakuti Ine Yehova sindisinthika, cifukwa cace inu ana a Yakobo simunathedwa.

7 Kuyambira masiku a makolo anu mwapambuka kuleka malemba anga osawasunga. Bwererani kudza kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu, ati Yehova wa makamu. Koma inu mukuti, Tibwerere motani?

8 Kodi munthu adzalanda za Mulungu? ndipo inu mundilanda Ine. Koma mukuti, Takulandani zotani? Limodzi limodzi la magawo khumi, ndi zopereka.

9 Mutembereredwa ndi temberero; pakuti mundilanda Ine, ndinu mtundu uwu wonse.

10 Mubwere nalo limodzi limodzi lonse la khumi, ku nyumba yosungiramo, kuti m'nyumba mwanga mukhale cakudya; ndipo mundiyese nako tsono, ati Yehova wa makamu, ngati sindikutsegulirani mazenera a kumwamba, ndi kukutsanulirani mdalitso wakuti adzasoweka malo akuulandira.

11 Ndipo ndidzadzudzula zolusa cifukwa ca inu, kuti zisakuonongereni zipatso za nthaka yanu; ngakhale mpesa wanu sudzayoyoka zipatso zace, zosaca m'munda, ati Yehova wa makamu.

12 Ndipo amitundu onse adzacha inu odala; pakuti mudzakhala dziko lokondweretsa, ati Yehova wa makamu.

13 Mau anu andilimbira, ati Yehova. Koma inu mukuti, Tanena motsutsana nanu ndi ciani?

14 Mwanena, Kutumikira Mulungu nkwa cabe; ndipo tapindulanji ndi kusunga udikiro wace, ndi kuyenda obvala zamaliro pamaso pa Yehova wa makamu?

15 Ndipo tsopano tiwacha odzikuza odala, inde iwo ocita zoipa amangidwa ngati nyumba; inde, ayesa Mulungu, napulumuka.

16 Pamenepo iwo akuopa Yehova analankhulana wina ndi mnzace; ndipo Yehova anawachera khutu namva, ndi buku la cikumbutso linalembedwa pamaso pace, la kwa iwo akuopa Yehova, nakumbukila dzina lace.

17 Ndipo adzakhala anga anga, ati Yehova wa makamu, tsiku ndidzaikalo, ndipo ndidzawaleka monga munthu aleka mwana wace womtumikira.

18 Pamenepo mudzabwera ndi kuzindikira pakati pa wolungama ndi woipa, pakati pa iye wotumikira Mulungu ndi iye wosamtumikira.

4

1 Pakuti taonani, likudza tsiku, lotentha ngati ng'anjo; ndipo onse akudzikuza ndi onse akucita coipa, adzakhala ngati ciputu; ndi tsiku lirinkudza lidzawayatsa, ati Yehova wa makamu, osawasiyira muzu kapena nthambi.

2 Koma inu akuopa dzina langa, dzuwa la cilungamo lidzakuturukirani, muli kuciritsa m'mapiko mwace; ndipo mudzaturuka ndi kutumphatumpha ngati ana a ng'ombe onenepa,

3 Ndipo mudzapondereza oipa; pakuti adzakhala ngati mapulusa ku mapazi anu, tsiku ndidzaikalo, ati Yehova wamakamu.

4 Kumbukilani cilamulo ca Mose mtumiki wanga, ndinamlamuliraco m'Horebu cikhale ca Israyeli lonse, ndico malemba ndi maweruzo.

5 Taonani, ndidzakutumizirani Eliya mneneri lisanadze tsiku lalikuru ndi loopsa la Yehova.

6 Ndipo adzabwezera mitima ya atate kwa ana, ndi mitima ya ana kwa atate ao; kuti ndisafike ndi kukantha dziko lionongeke konse.