1

1 PAULO a mtumwi wa Kristu Yesu mwa cifuniro ca Mulungu, monga mwa lonjezano la moyo wa m'Kristu Yesu,

2 kwa Timoteo, mwana wanga wokondedwa: Cisomo, cifundo, mtendere za kwa Mulungu Atate ndi Kristu Yesu Ambuye wathu.

3 Ndiyamika Mulungu, amene ndimtumikira kuyambira makolo anga ndi cikumbu mtima coyera, kuti ndikumbukila iwe kosalekeza m'mapemphero anga,

4 pokhumba usiku ndi usana kukuona iwe, ndi kukumbukila misozi yako, kuti ndidzazidwe naco cimwemwe;

5 pokumbukila cikhulupiriro cosanyenga ciri mwa iwe, cimene cinayamba kukhala mwa mbuye wako Loisi, ndi mwa mai wako Yunike, ndipo, ndakopeka mtima, mwa iwenso.

6 Cifukwa cace ndikukumbutsa iwe ukoleze mphatso ya Mulungu, iri mwa iwe mwa kuika kwa manja anga,

7 Pakuti Mulungu sanatipatsa mzimu wa mantha; komatu wa mphamvu ndi cikondi ndi cidziletso.

8 Potero usacite manyazi pa umboni wa Ambuye wathu, kapena pa ine wandende wace; komatu umve masautso ndi Uthenga Wabwino, monga mwa mphamvu ya Mulungu;

9 amene anatipulumutsa ife, natiitana ife ndi maitanidwe oyera, si monga mwa nchito zathu, komatu monga mwa citsimikizo mtima ca iye yekha, ndi cisomo, copatsika kwa ife mwa Kristu Yesu zisanayambe nthawi zoyamba,

10 koma caonetsedwa tsopano m'maonekedwe a Mpulumutsi wathu Kristu Yesu, amenedi anatha imfa, naonetsera poyera moyo ndi cosabvunda mwa Uthenga Wabwino,

11 umene ndaikikapo mlaliki, ndi mtumwi ndi mphunzitsi wace.

12 Cifukwa ca ideo ndinamva zowawa izi; komatu sindicita manyazi; pakuti ndimdziwa iye amene ndamkhulupirira, ndipo ndikopeka mtima kuti ali wa mphamvu ya kudikira cosungitsa eangaeo kufikira tsiku lijalo.

13 Gwira citsanzo ca mau a moyo, amene udawamva kwa ine, mwa cikhulupiriro ndi cikondi ciri mwa Kristu Yesu.

14 Cosungitsa cokomaca udikire mwa Mzimu Woyera amene akhalitsa mwa ife.

15 Ici ucidziwa, kuti onse a m'Asiya adabwerera kusiyana nane; a iwo ali Fugelo ndi Hermogene,

16 Ambuye acitire banja la Onesiforo cifundo; pakuti anatsitsimutsa ine kawiri kawiri, ndipo sanacita manyazi ndi unyolo wanga;

17 komatu pokhala m'Roma iye anandifunafuna ine ndi khama, nandipeza,

18 (Ambuye ampatse iye apeze cifundo ndi Ambuye tsiku lijalo); ndi muja ananditumikira m'zinthu zambiri m'Efeso, uzindikira iwe bwino.

2

1 Ndipo iwe, mwana wanga, limbika m'cisomo ca m'Kristu Yesu.

2 Ndipo zimene wazimva kwa ine mwa mboni zambiri, zomwezi uikize kwa anthu okhulupirika, amene adzadziwa kuphunzitsa enanso.

3 Umve zowawa pamodzi nane monga msilikari wabwino wa Kristu Yesu.

4 Msilikari sakodwa nazo nchito wamba, kuti akakondweretse iye amene adamlemba usilikari.

5 Koma ngatinso wina ayesana nao m'makani a masewero, sambveka korona ngati sanayesana monga adapangana.

6 Wam'munda wogwiritsitsa nchitoyo ayenera akhale woyamba kulandira zipatsozoo

7 Lingirira cimene ndinena; pakuti Ambuye adzakupatsa cidziwitso m'zonse.

8 Kumbukila Yesu Kristu, wouka kwa akufa, wocokera m'mbeu ya Davide, monga mwa Uthenga Wabwino wanga;

9 m'menemo ndimva zowawa kufikira zomangira, monga wocita zoipa; koma mau a Mulungu samangika.

10 Mwa ici ndipirira zonse, cifukwa ca osankhika, kuti iwonso akapeze cipulumutsoeo ca mwa Kristu Yesu, pamodzi ndi ulemerero wosatha.

11 Okhulupirika mauwa: Pakuti ngati tidamwalira ndi iye, tidzakhalanso moyo ndi iye:

12 ngati ttpirira, tidzacitanso ufumu ndi iye: ngati timkana Iye, Iyeyunso adzatikana ife:

13 ngati tikhala osakhulupirika, Iyeyu akhala wokhulupirika; pakuti sakhoza kudzikana yekha.

14 Uwakumbutse izi, ndi kuwacitira umboni pamaso pa Ambuye, kuti asacite makani ndi mau osapindulitsa kanthu, koma ogwetsa iwo akumva.

15 Ucite cangu kudzionetsera kwa Mulungu wobvomerezeka, wanchito wopanda cifukwa ca kucita manyazi, wolunjika nao bwino mau a coonadi.

16 Koma pewa nkhani zopanda pace; pakuti adzapitirira kutsata cisapembedzo,

17 ndipo mau ao adzanyeka cironda; a iwo ali Humenayo ndi Fileto;

18 ndiwo amene adasokera kunena za coonadi, ponena kuti kuuka kwa akufa kwacitika kale, napasula cikhulupiriro ca ena.

19 Koma ndithu maziko a Mulungu aimika pokhazikika, ndi cukhala naco cizindikilo ici, Ambuye azindikira iwo amene ali ace; ndipo, Adzipatule kwa cosalungama yense wakuehula dzina la Ambuye.

20 Koma m'nyumba yaikuru simuli zotengera za golidi ndi siliva zokha, komatunso za mtengo ndi dothi; ndipo zina zaulemu, koma zina zopanda ulemu.

21 Ngati tsono munthu adziyeretsa yekha pa izi, adzakhala cotengera ca kuulemu, copatulidwa, coyenera kucita naco Mbuye, cokonzera nchito yonse yabwino.

22 Koma thawa zilakolako za unyamata, nutsate cilungamo, cikhulupiriro, cikondi, mtendere, pamodzi ndi iwo akuitana pa Ambuye ndi mitima yoyera.

23 Koma mafunso opusa ndi opanda malango upewe, podziwa kuti abala ndeu.

24 Ndipo kapolo wa Ambuye sayenera kucita ndeu, komatu akhale woyenera, waulere pa onse, wodziwa kuphunzitsa, woleza,

25 1 wolangiza iwo akutsutsana mofatsa; 2 ngati kapena Mulungu awapatse iwo citembenuziro, kukazindikira coonadi,

26 ndipo 3 akadzipulumutse ku msampha wa mdierekezi, m'mene anagwidwa naye, ku cifuniro cace.

3

1 Koma zindikira ici, kuti masiku otsiriza zidzafika nthawi zowawitsa.

2 Pakuti anthu adzakhala odzikonda okha, okonda ndarama, odzitamandira, odzikuza, amwano, osamvera akuwabala, osayamika,

3 osayera mtima, opanda cikondi cacibadwidwe, osayanjanitsika, akudierekeza, osakhoza kudziletsa, aukali, osakonda abwino,

4 aciwembu, aliuma olimbirira, otukumuka mtima, okonda zokondweretsa munthu, osati okonda Mulungu;

5 akukhala nao maonekedwe a cipembedzo, koma mphamvu yace adaikana; kwa iwonso udzipatule,

6 Pakuti mwa iwo akhala akukwawira m'nyumba, nagwira akazi opusa, osenza akatundu a zoipa zao, otengedwa nazo zilakolako za mitundu mitundu:

7 ophunzira nthawi zonse, koma sakhoza konse kufikira ku cizindikiritso ca coonadi.

8 Ndipo monga momwe Yane ndi Yambre anatsutsana naye Mose, kotero iwonso atsutsana naco coonadi; ndiwo anthu obvunditsitsa mtima, osatsimikizidwa pacikhulupiriro.

9 Koma sadzapitirirapo; pakuti kupusa kwao kudzaonekeratu kwa onse, monganso kupusa kwa iwo aja.

10 Koma iwe watsatatsata ciphunzitso canga, mayendedwe, citsimikizo mtima, cikhulupiriro, kuleza mtima, cikondi, cipiriro,

11 mazunzo, kumva zowawa; zotere zonga anandicitira m'Antiokeya, m'Ikoniya, m'Lustro, mazunzo otere onga ndawamva; ndipo m'zonsezi Ambuye anandilanditsa.

12 Ndipo onse akufuna kukhala opembedza m'moyo mwa Kristu Yesu, adzamva mazunzo.

13 Koma anthu oipa ndi onyenga, adzaipa ciipire, kusokeretsa ndi kusokeretsedwa.

14 Koma ukhalebe iwe mu izi zimene waziphunzira, nutsimikizika mtima nazo, podziwa amene adakuphunzitsa;

15 ndi kuti kuyambira ukhanda wako wadziwa malembo opatulika, okhoza kukupatsa nzeru kufikira cipulumutso, mwa cikhulupiriro ca mwa Kristu Yesu.

16 Lemba liri lonse adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa ciphunzitso, citsutsano, cikonzero, cilangizo ca m'cilungamo:

17 kuti munthu wa Mulungu akhale woyenera, wokonzeka kucita nchito iri yonse yabwino.

4

1 Ndikucitira umboni pamaso pa Mulungu ndi Kristu Yesu, amene adzaweruza amoyo ndi akufa, ndi pa maonekedwe ace ndi ufumu wace;

2 lalikira mau; cita nao pa nthawi yace, popanda nthawi yace; tsutsa, dzudzula, cenjeza, ndi kuleza mtima konse ndi ciphunzitso.

3 Pakuti idzafika nthawi imene sadzalola ciphunzitso colamitsa; komatu poyabwa m'khutu adzadziuniikitsa aphunzitsi monga mwa zilakolako za iwo okha:

4 ndipo adzalubza dala pacoonadi, nadzapatukira kutsata nthanu zacabe.

5 Koma iwe, khala maso m'zonse, imva zowawa, cita nchito ya mlaliki wa Uthenga Wabwino, kwaniritsa utumiki wako.

6 Pakuti ndirimkuthiridwa nsembe tsopano, ndipo nthawi ya kumasuka kwanga yafika.

7 Ndalimbana nako kulimbana kwabwino, ndatsiriza njirayo, ndasunga cikhulupiriro:

8 cotsalira wandiikira ine korona wa cilungamo, amene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa ine tsiku lijalo: ndipo si kwa ine ndekha, komatunso kwa onse amene anakonda maonekedwe ace.

9 Tayesetsa kudza kwa ine msanga:

10 pakuti Dema wandisiya ine, atakonda dziko lino lapansi, napita ku Tesalonika; Kresike ku Galatiya, Tito ku Dalimatiya.

11 Luka yekha ali pamodzi ndi ine. Umtenge Marko, adze pamodzi ndi iwe; pakuti ayenera kunditumikira.

12 Koma Tukiko ndamtuma ku Efeso.

13 Copfunda cija ndinacisiya ku Trowa kwa Karpo, udze naco pakudza iwe, ndi mabuku, makamaka zikopa zija zolembedwa.

14 Alesandro wosula mkuwa anandicitira zoipa zambiri: adzambwezera iye Ambuye monga mwa nchito zace;

15 ameneyo iwenso ucenjere naye; pakuti anatsutsana nao mau athu.

16 Pa codzikanira canga coyamba panalibe mmodzi anandithangata, koma onse anandisiya; cimeneco cisawerengedwe cowatsutsa.

17 Koma Ambuye anaima nane nandipatsa mphamvu; kuti mwa ine cilalikiro cimveke konse konse, ndi amitundu onse amve; ndipo ndinalanditsidwa m'kamwa mwa mkango.

18 Ambuye adzandilanditsa ku nchito yonse yoipa, nadzandipulumutsa ine kulowa Ufumu wace wa Kumwamba; kwa iye ukhale ulemerero ku nthawi za nthawi. Amen.

19 Lankhula Priska ndi Akula, ndi banja la Onesiforo.

20 Erasto anakhalira m'Korinto; koma Trofimo ndamsiya wodwala ku Mileto.

21 1 Tayesetsa kudza isanadze nyengo yacisanu. Akulankhula iwe Eubulo, ndi Pude, ndi Lino, ndi Klaudiya, ndi abale onse.

22 2 Ambuye akhale ndi mzimu wako. Cisomo cikhale nanu.