1 PACIYAMBI panali Mau, ndipo Mau anali kwa Mulungu, ndipo Mau ndiye Mulungu.
2 Awa anali paciyambi kwa Mulungu,
3 Zonse: zinalengedwa ndi iye; ndipo kopanda iye sikunalengedwa kanthu kali konse kolengedwa,
4 Mwa iye munali moyo; ndi moyowu unali kuunika kwa anthu.
5 Ndipo kuunikaku kunawala mumdima; ndi mdimawu sunakuzindikira.
6 Kunali munthu, wotumidwa ndi Mulungu, dzina lace ndiye Yohane.
7 Iyeyu anadza mwa umboni kudzacita umboni za kuunikaku, kuti onse akakhulupirire mwa iye,
8 iye sindiye kuunikaku, koma anatumidwa kukacita umboni wa kuunikaku.
9 Uku ndiko kuunika kweni kweni, kumene kuunikira anthu onse akulowa m'dziko lapansi.
10 Anali m'dziko lapansi, ndi dziko linalengedwa ndi iye, koma dziko silinamzindikira iye.
11 Anadza kwa zace za iye yekha, ndipo ace a mwini yekha sanamlandira iye.
12 Koma onse amene anamlandira iye, kwa iwo anapatsa mphamvu yakukhala ana a Mulungu, kwa iwotu, akukhulupirira dzina lace;
13 amene sanabadwa ndi mwazi, kapena ndi cifuniro ca thupi, kapena ndi cifuniro ca munthu, koma ca Mulungu.
14 Ndipo Mau anasandulika thupi, nakhazikika pakati pa ife, ndipo tinaona ulemerero wace, ulemerero wonga wa wobadwa yekha wa Atate, wodzala ndi cisomo ndi coonadi.
15 Yohane acita umboni za iye, napfuula nati, Uyu ndiye amene ndinanena za iye, Wakudzayo pambuyo panga analipo ndisanabadwe ine; cifukwa anakhala woyamba wa ine.
16 Cifukwa mwa kudzala kwace tinalandira ife tonse, cisomo cosinthana ndi cisomo.
17 Cifukwa cilamulo cinapatsidwa mwa Mose; cisomo ndicoonadi zinadza mwa Yesu Kristu.
18 Kulibe munthu anaona Mulungu nthawi zonse; Mwana wobadwa yekha wakukhala pa cifuwa ca Atate, Iyeyu anafotokozera.
19 Ndipo umene ndiwo umboni wa Yohane, pamene Ayudaanatuma kwa iye ansembe ndi alembi a ku Yerusalemu akamfunse iye, Ndiwe yani?
20 Ndipo anabvomera, wosakana; nalola kuti, Sindine Kristu.
21 Ndipo anamfunsa iye, Nanga bwanji? ndiwe Eliya kodi? Nanena iye, Sindine iye, Ndiwe Mneneriyo kodi? Nayankha, Iai.
22 Cifukwa cace anati kwa iye, Ndiwe yani? kuti tibwezere mau kwa iwo anatituma ife. Unena ciani za iwe wekha?
23 Anati, 1 Ndine mau a wopfuula m'cipululu, Lungamitsani njira ya Mbuye, monga anati Yesaya mneneriyo.
24 Ndipo otumidwawo analia kwa Marisi.
25 Ndipo anamfunsa iye, nati kwa iye, Koma ubatiza bwanji, ngati suli Kristu, kapena Eliya, kapena Mneneriyo?
26 Yohane anawayankha, nati, 2 Ine ndibatiza ndi madzi; pakati pa inu paimirira amene simumdziwa,
27 3 ndiye wakudza pambuyo panga, amene sindiyenera kummasulira lamba la nsapato yace.
28 Zinthu izi zinacitika m'Betaniya tsidya lija la Y ordano, pomwe analikubatiza Yohane.
29 M'mawa mwace anaona Yesu alinkudza kwa iye, nanena, 4 Onani Mwanawankhosa wa Mulungu 5 amene acotsa cimo lace la dziko lapasi!
30 6 Ndiye amene ndinati za iye, Pambuyo panga palinkudza munthu amene analipo ndisanabadwe ine; pakuti anali woyamba wa ine.
31 Ndipo sindinamdziwa iye; koma kuti aonetsedwe kwa Israyeli, 7 cifukwa ca ici ndinadzaine kudzabatiza ndi madzi.
32 Ndipo Yohane anacita umboni, nati, 8 Ndinaona Mzimu alikutsika kucokera Kumwamba monga nkhunda; nakhalabe pa iye.
33 Ndipo sindinamdziwa iye, koma wonditumayo kudzabatiza ndi madzi, Iyeyu ananena ndi ine, Amene udzaona Mzimu atsikira, nakhala pa iye, 9 yemweyu ndiye wakubatiza ndi Mzimu Woyera.
34 Ndipo ndaona ine, ndipo ndacita umboni kuti Mwana wa Mulungu ndi Yemweyu.
35 M'mawa mwacenso analikuimirira Yohane ndi awiri a akuphunzira ace;
36 ndipo poyang'ana Yesu alikuyenda, anati, 10 Onani Mwanawankhosa wa Mulungu!
37 Ndipo akuphunzira awiriwo anamva iye alinkulankhula, natsata Yesu.
38 Koma Yesu anaceuka, napenya iwo alikumtsata, nanena nao, Mufuna ciani? Ndipo anati kwa iye, Rabi (ndiko kunena posandulika, Mphunzitsi), mukhala kuti?
39 Nanena nao, Tiyeni, mukaone, Pamenepo anadza naona kumene anakhala; nakhala ndi iye tsiku lomwelo; panali monga ora lakhumi.
40 Andreya mbale wace wa Simoni Petro anali mmodzi wa awiriwo, anamva Yohane, namtsata iye.
41 Anayamba iye kupeza mbale wace yekha Simoni, nanena naye, Tapeza ife Mesiya (ndiko kusandulika Kristu).
42 Anadza naye kwa Yesu. M'mene anamyang'ana iye, anati, Uli Simoni mwana wa Yohane; 11 udzachedwa Kefa (ndiko kusandulika Petro).
43 M'mawa mwace anafuna kuturuka kunka ku Galileya, napeza Filipo, Ndipo Yesu ananena naye, Tsata Ine.
44 Koma Filipo anali wa ku Betsaida, mudzi wa Andreya ndi Petro.
45 Filipo anapeza Natanayeli, nanena naye, iye 12 amene Mose analembera za iye m'cilamulo, ndi aneneri, tampeza, ndiye Yesu mwana wa Yosefe wa ku Nazarete.
46 Natanayeli anati kwa iye, 13 Ku Nazarete nkutha kucokera kanthu kabwino kodi? Filipo ananena naye, Tiye ukaone.
47 Yesu anaona Natanayeli alinkudza kwa iye, nanena za iye, Onani, M-israyeli ndithu, mwa iye mulibe cinyengo!
48 Natanayeli ananena naye, Munandidziwira kuti? Yesu anayankha nati kwa iye, Asanakuitane Filipo, pokhala iwe pansi pa mkuyu paja, ndinakuona iwe.
49 Natanayeli anayankha Iye, Rabi, 14 Inu ndinu Mwana wa Mulungu, 15 ndinu Mfumu ya Israyeli,
50 Yesu anayankha nati kwa iye, Cifukwa ndinati kwa iwe kuti ndinakuona pansi pa mkuyu ukhulupirira kodi? udzaona zoposa izi.
51 Ndipo ananena naye, Indetu, indetu, ndinena ndi Inu, 16 Mudzaona thambo lotseguka, ndi angeloa Mulungu akwera natsikira pa Mwana wa munthu.
1 Ndipo tsiku lacitatu pariali ukwati m'Kana wa m'Galileya; ndipo amace wa Yesu anali komweko.
2 Ndipo Yesu yemwe ndi akuphunzira ace anaitanidwa ku ukwatiwo.
3 Ndipo pakutha vinyo, amace wa Yesu ananena naye, Alibe vinyo,
4 Yesu nanena naye, Mkazi, ndiri ndi ciani ndi inu? nthawi yanga siinafike.
5 Amace ananena kwa atumiki, Cimene ciri conse akanena kwa inu, citani.
6 Ndipopanali pamenepo mitsuko yamiyala isanu ndi umodzi yoikidwako monga mwa mayeretsedwe a Ayuda, yonse ya miyeso iwiri kapena itatu.
7 Yesu ananena nao, Dzazani mitsukoyo ndi madzi. Naidzaza, nde nde nde.
8 Ndipo ananena nao, Tungani tsopano, mupite nao kwamkulu wa phwando. Ndipo anapita nao.
9 Koma pamene mkuluyo analawa madzi osanduka vinyowo, ndipo sanadziwa kumene anacokera (koma atumiki amene adatiinga madzi anadziwa), mkuluyo anaitana mkwati,
10 nanena naye, Munthu ali yense amayamba kuika vinyo wokoma; ndipo anthu atamwatu, pamenepo wina wosakoma; koma iwe wasunga vinyo wokoma kufikira tsopano lino.
11 Ciyambi ici ca zizindikilo zace Yesu anacita m'Kana wa m'Galileya naonetsera ulemerero wace; ndipo akuphunzira ace anakhulupirira iye.
12 Zitapita izianatsikira ku Kapemao, iye ndi amace, ndiabale ace, ndi ophunzira ace; nakhala komweko masiku owerengeka.
13 Ndipo Paskha wa Ayuda unayandikira, ndipo Yesu anakwera kunka ku Yerusalemu.
14 Ndipo anapeza m'Kacisiiwo akugulitsa ng'ombe ndi nkhosa ndi nkhunda, ndi akusinthana ndalama alikukhala pansi.
15 Ndipo pamene adapanga mkwapulo wazingwe, anaturutsa onse m'Kacisimo, ndi nkhosa ndi ng'ombe; nakhuthula ndalama za osinthanawo, nagubuduza magome;
16 nati kwa iwo akugulitsa nkhunda, Cotsani izi muno; musamayesa nyumba ya Atate wanga nyumba ya malonda.
17 Akuphunzira ace anakumbukila kuti kunalembedwa, Cangu ca pa nyumba yanu candidya ine.
18 Cifukwa cace Ayuda anayankha nati kwa iye, Mutionetsera ife cizindikilo canji, pakuti mucita izi?
19 Yesu anayankha nati kwa iwo, Pasulani kacisi uyu, ndipo masiku atatu ndidzamuutsa.
20 Pamenepo Ayuda anati, Zaka makumi anai ndi zisanu ndi cimodzi analimkumanga Kacisiyu, kodi inu mudzamuutsa masiku atatu?
21 Koma iye analikunena za kacisi wathupi lace.
22 Cifukwa cace atauka kwa akufa, akuphunzira ace anakumbukira kuti ananena ici; ndipo anakhulupirira colemba, ndi mau amene Yesu ananena.
23 Koma pamene anali m'Yerusalemu pa Paskha paphwando, ambiri anakhulupirira dzinalace, pakuona zizindikilo zace zimene anaeitazi.
24 Koma Yesu sanakhulupirira iwo kuti akhale nao, cifukwa iye anadziwa anthu onse,
25 ndipo sanasowa wina acite umboni za munthu; pakuti anadziwa iye yekha cimene cinali mwa munthu.
1 Koma panali munthu wa Afarisi, dzina lace Nikodemo, mkulu wa Ayuda,
2 Iyeyu anadza kwa Yesu usiku, nati kwa iye, Rabi, tidziwa kuti Inu ndinu mphunzitsi wocokera kwa Mulungu; pakuti palibe munthu akhoza kucita zizindikilo zimene inu mucita, ngati Mulungu sakhala naye,
3 Yesu anayankha nati kwa iye, Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, Ngati munthu sabadwa mwatsopano, sakhoza kuona Ufumu wa Mulungu.
4 Nikodemoananena kwa iye, Munthu akhoza bwanji kubadwa atakalamba? Kodi akhoza kulowanso m'mimba ya amace ndi kubadwa?
5 Yesu anayankha, Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, Ngati munthu sabadwa mwa madzi ndi Mzimu, sakhoza kulowa ufumu wa Mulungu.
6 Cobadwa m'thupi cikhala thupi, ndipo cobadwa mwa Mzimu, cikhala mzimu.
7 Usadabwe cifukwa ndinati kwa iwe, Uyenera kubadwa mwatsopano.
8 Mphepo iomba pomwe ifuna, ndipo ukumva mau ace, komavsudziwa, kumene icokera, ndi kumene imuka; cotero ali yense wobadwa mwa Mzimu.
9 Nikodemo anayankha nati kwa iye, Izi zingatheke bwanji?
10 Yesu anayankha nati kwa iye, Kodi uli mphunzitsi wa Israyeli, ndipo sudziwa izi?
11 Indetu, indetu, ndinena kwa iwe, Tilankhula cimene ticidziwa, ndipo ticita umboni za cimene taeiona; ndipo umboni wathu simuulandira.
12 Ngati ndakuuzani za pansi pano, ndipo simukhulupira, mudzakhulupira bwanji, ngati ndikuuzani za Kumwamba?
13 Ndipo kulibe munthu anakwera Kumwamba, koma iye wotsikayo kucokera Kumwamba, ndiye Mwana wa munthu, wokhala m'Mwambayo.
14 Ndipo monga Mose anakweza njoka m'cipululu, cotero Mwana wa munthu ayenera kukwezedwa;
15 kuti yense wakukhulupira akhale nao moyo wosatha mwa iye.
16 Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wace wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha.
17 Pakuti Mulungu sanatuma Mwana wace ku dziko lapansi, kuti akaweruze dziko lapansi, koma kuti dziko lapansi likapulumutsidwe ndi iye.
18 Wokhulupirira Iye saweruzidwa; wosakhulupira waweruzidwa ngakhale tsopano, cifukwa sanakhulupirira dzina la Mwana wobadwa yekha wa Mulungu.
19 Koma ciweruziro ndi ici, kuti kuunika kunadza ku dziko lapansi, ndipo anthu anakonda mdima koposa kuunika; pakuti nchito zao zinali zoipa.
20 Pakuti yense wakucita zoipa adana nako kuunika, ndipo sakudza kwa kuunika, kuti zingatsutsidwe nchito zace.
21 Koma wocita coonadi adza kukuunika, kuti nchito zace zionekere kuti zinacitidwa mwa Mulungu.
22 Zitapita in anadza Yesu ndi akuphunzira ace ku dziko la Yudeya; ndipo pamenepo anatsotsa nao pamodzi, nabatiza.
23 Ndipo Yohane analinkubatiza m'Ainoni pafupi pa Salemu, cifukwa panali madzi ambiri pamenepo; ndipo analinkufikako anthu, nalinkubatizidwa.
24 Pakuti Yohane sanaikidwe m'ndende.
25 Pamenepo padauka kufunsana mwa ophunzira ace a Yohane ndi Myuda za mayeretsedwe.
26 Ndipo anadza kwa Yohane, nati kwa iye, Rabi, Iye amene anali ndi inu tsidya lija la Y ordano, amene munamcitira umboni, taonani yemweyu abatiza, ndipo anthu onse alinkudza kwa iye.
27 Yohane anayankha nati, Munthu sakhoza kulandira kanthu, ngati sikapatsidwa kwa iye kocokera Kumwamba.
28 Inu nokha mundicitira umboni, kuti ndinati, Sindine Kristu, koma kuti ndiri wotumidwa m'tsogolo mwace mwa iye.
29 Iye amene ali naye mkwatibwi ali mkwati, koma mnzace wa mkwatiyo, wakuimirira ndi kumvera iye, akondwera kwakukuru cifukwa ca mau a mkwatiyo; cifukwa cace cimwemwe canga cimene cakwanira.
30 Iyeyo ayenera kukula koma ine ndicepe.
31 Iye wocokera Kumwamba ali woposa onse; iye amene ali wa dziko lapansi ali wa dziko lapansi, nalankhula za dziko lapansi: Iye wocokera Kumwamba ali woposa onse.
32 Cimene anaciona nacimva, acita umboni wa ici comwe; ndipo kulibe munthu alandira umboni wace.
33 1 Iye amene analandira umboni wace anaikapo cizindikilo cace kuti Mulungu ali woona.
34 Pakuti 2 Iye amene Mulungu anamtuma alankhula mau a Mulungu; pakuti 3 sapatsa Mzimu ndi muyeso.
35 4 Atate akonda Mwana, nampatsa zinthu zonse m'dzanja lace.
36 Iye amene akhulupirira Mwanayo ali nao moyo wosatha; koma iye amene sakhulupirira Mwanayo sadzaona moyo, koma mkwiyo wa Mulungu ukhala pa iye.
1 Cifukwa cace pamene Ambuye anadziwa kuti Afarisi adamva kuti Yesu anayesa anthu ophunzira, nawabatiza koposa Yohane
2 (angakhale Yesu sanabatiza yekha koma ophunzira ace),
3 anacokera ku Yudeya, namukanso ku Galileya.
4 Ndipo anayenerakupita pakati pa Samariya.
5 Cifukwa cace anadza ku mudzi wa Samariya, dzina lace Sukari, pafupi pa kadziko kamene Yakobo adapatsa mwana wace Yosefe;
6 ndipo pamenepo panali citsime ca Yakobo. Ndipo Yesu, popeza analema ndi ulendo wace, motero anakhala pacitsime,
7 Kunali ngati ora lacisanu ndi cimodzi. Kunadza mkazi woturuka m'Samariya kudzatunga madzi. Yesu ananena naye, Undipatse Ine ndimwe.
8 Pakuti ophunzira ace adacoka kunka kumudzi kuti akagule cakudya.
9 Pamenepo mkazi wa m'Samariya ananena ndi iye, Bwanji Inu, muli Myuda, mupempha kwa ine kumwa, ndine mkazi Msamariya? (pakuti Ayuda sayenderana nao Asamariya),
10 Yesu anayankha nati kwa iye, Ukadadziwa mtulo wa Mulungu, ndi Iye amene alinkunena ndi iwe, Undipatse Ine ndimwe; ukadapempha iye, ndipo akadakupatsa madzi amoyo.
11 Mkaziyo ananena ndi Iye, Ambuye, mulibe cotungira madzi, ndi citsime ciri cakuya; ndipo mwatenga kuti madzi amoyo?
12 kodi muli wamkuru ndi atate wathu Yakobo amene anatipatsa ife citsimeci, namwamo iye yekha, ndi ana ace, ndi zoweta zace?
13 Yesu anayankha nati kwa iye, Yense wakumwako madzi awa adzamvanso Iudzu;
14 koma iye wakumwa madzi amene Ine ndidzampatsa sadzamva ludzu nthawi zonse; koma madzi amene Ine ndidzampatsa adzakhala mwa iye kasupe wa madzi otumphukira ku moyo wosatha.
15 Mkaziyo ananena kwa iye, Ambuye, ndipatseni madzi amene, kuti ndisamve ludzu, kapena ndisadze kuno kudzatunga.
16 Yesu ananena kwa iye, Muka, kamuitane mwamuna wako, nudze kuno.
17 Mkazi anayankha nati kwa iye, Ndiribe mwamuna. Yesu ananena naye, Wanena bwino, kuti mwamuna ndiribe;
18 pakuti wakhala nao amuna asanu; ndipo iye amene ukhala nave tsopano sali mwamuna wako; ici wanena zoona.
19 Mkazi ananena ndi iye, Ambuye, ndizindikira kuti muli Mneneri.
20 Makolo athu analambira m'phiri ili; ndipo inu munena, kuti m'Yerusalemu muli malo ozenera kulambiramo anthu.
21 Yesu ananena naye, Tamvera Ine, mkazi iwe, kuti ikudza nthawi, imene simudzalambira Atate kapena m'phiri ili, kapena m'Yerusalemu.
22 Inu mulambira cimene simucidziwa; ife tilambira cimene ticidziwa; pakuti cipulumutso cicokera kwa Ayuda.
23 Koma ikudza nthawi, ndipo tsopano iripo, imene olambira oona adzalambira Atate mumzimu ndi m'coonadi; pakuti Atate afuna otere akhale olambira ace.
24 Mulungu ndiye mzimu; ndipo omlambira iye ayenera kumlambira mumzimu ndi m'coonadi.
25 Mkazi ananena ndi Iye, Ndidziwa kuti Mesiya adza (wochedwa Kristu): akadzadza Iyeyu, adzatiuza zonse.
26 Yesu ananena naye, Ine wakulankhula nawe ndine amene.
27 Ndipo pamenepo anadza ophunzira ace; nazizwa kuti analinkulankhula ndi mkazi; koma panalibe wina anati, Mufuna ciani? kapena, mulankhula naye ciani?
28 Pamenepo mkazi anasiya mtsuko wace, namuka kumudzi, nanena ndi anthu,
29 Tiyeni, mukaone munthu, amene anandiuza zinthu ziri zonse ndinazicita: ameneyu sali Kristu nanga?
30 Anaturuka iwo m'mudzi ndipo analinkudza kwa iye.
31 Pa mphindikati iyi ophunzira ace anampempha iye, ndi kunena, Rabi, idyani.
32 Koma iye anati kwa iwo, Ine ndiri naco cakudya cimene inu simucidziwa.
33 Cifukwa cace ophunzira ananena wina ndi mnzace, Kodi pali wina anamtengera iye kanthu kakudya?
34 Yesu ananena nao, Cakudya canga ndico kuti ndicite cifuniro ca iye amene anandituma Ine, ndi kutsiriza nchito yace.
35 Kodi simunena inu, kuti, Yatsala miyezi inai, ndipo kudza kumweta? Onani ndinena kwa inu, Kwezani maso anu, nimuyang'ane m'minda, kuti mwayera kale kufikira kumweta.
36 Wakumweta alandira kulipira, nasonkhanitsira cobala ku moyo wosatha; kuti wofesayo akakondwere pamodzi ndi womwetayo.
37 Pakuti m'menemo conenaco ciri coona, Wofesa ndi wina, womweta ndi winanso.
38 Ine ndinatuma inu kukamweta cimene simunagwirirapo nchito: ena anagwira nchito, ndipo inu mwalowa nchito yao.
39 Ndipo m'mudzi mula anthu Asamariya ambiri anamkhulupirira iye cifukwa ca mau a mkazi, wocita umboniyo, kuti, Anandiuza ine zinthu ziri zonse ndinazicita.
40 Cifukwa cace pamene Asamariya anadza kwa iye, anamfunsa akhale nao; ndipo anakhala komweko masiku awiri.
41 Ndipo ambiri oposa anakhulupira cifukwa ca mau ace:
42 ndipo ananena kwa mkazi, kuti, Tsopano sitikhulupira cifukwa ca kulankhula kwako: pakuti tamva tokha, ndipo tidziwa kuti Mpulumutsi wa dziko lapansi ndi Iyeyu ndithu.
43 Koma atapita masiku awiriwo anacoka komweko kunka ku Galileya.
44 Pakuti Yesu mwini anacita umboni kuti, Mneneri alibe ulemu m'dziko la kwao.
45 Cifukwa cace pamene anadza ku Galileya, Agalileva anamlandira iye, atakaona zonse zimene anazicita m'Yerusalemu paphwando; pakuti iwonso ananka kuphwando.
46 Cifukwa cace Yesu anadzanso ku Kana wa m'Galileya, kumene anasandutsa madzi vinyo. Ndipo kunalimkulu wina wa mfumu, mwana wace anadwala m'Kapernao.
47 Iyeyu, pamene anamva kuti Yesu wacokera ku Yudeya nafika ku Galileya, ananka kwa iye, nampempha kuti atsike kukaciritsa mwana wace; pakuti anali pafupi imfa.
48 Pamenepo Yesu anati kwa iye, Ngati simuona zizindikilo ndi zozizwa, simudzakhulupira.
49 Mkuluyo ananena kwa iye, Ambuye, tsikani asanafe mwana wanga.
50 Yesu ananena naye, Muka, mwana wako ali ndi moyo, Munthuyo anakhulupirira mau amene Yesu anatero naye, namuka.
51 Ndipo m'mene analikutsika, akapolo ace anakomana, naye, nanena, kuti, Mwana wanu ali ndi moyo.
52 Cifukwa cace anawafunsa ora lace anayamba kuciralo. Pamenepo anati kwa iye, kuti, Dzulo, ora lacisanu ndi ciwiri malungo anamsiya.
53 Cifukwa cace atateyo anadziwa kuti ndi ora lomwelo limene Yesu anati kwa iye, Mwana wako ali ndi moyo; ndipo anakhulupira iye yekha ndi a pa banja lace onse.
54 Ici ndi cizindikilo caciwiri Yesu anacita, ataeokera ku Yudeya, ndi kulowa m'Galileya.
1 Zitapita izi panali phwando la Ayuda; ndipo Yesu anakwera kunka ku Yerusalemu.
2 Koma pali thamanda m'Yerusalemu pa cipata ca nkhosa, lochedwa m'Cihebri Betesda, liri ndi makumbi asanu.
3 M'menemo munagona khamu lalikuru la anthu odwala akhungu, opunduka miyendo, opuwala. [
4 ]
5 Koma panali munthu wina apo, ali m'kudwala kwace zaka makumi atatu kudza zisanu ndi zitatu.
6 Yesu, pakuona ameneyo alikugona, ndipo anadziwa kuti anatero nthawi yaikuru pamenepo, ananena naye, Ufuna kuciritsidwa kodi?
7 Wodwalayo anayankha, Ambuye, ndiribe wondibvika ine m'thamanda, pali ponse madzi abvundulidwa; koma m'mene ndirinkudza ine, wina atsika ndisanatsike ine.
8 Yesu ananena naye, Tauka, yalula mphasa yako, nuyende,
9 Ndipo pomwepo munthuyu anacira, nayalula mphasa yace, nayenda. Koma tsiku lomwelo linali la Sabata.
10 Cifukwa cace Ayuda ananena kwa wociritsidwayo, Ndi Sabata, ndipo sikuloledwa kwa iwe kuyalula mphasa yako.
11 Koma iyeyu anayankha iwo, iye amene anandiciritsa, yemweyu anati kwa ine, Yalula mphasa yako, nuyende,
12 Anamfunsa, Munthuyo ndani wonena ndi iwe, Yalula mphasa yako, nuyende?
13 Koma wociritsidwayo sanadziwa ngati ndani; pakuti Yesu anacoka kacetecete, popeza panali anthu aunyinji m'malo muja.
14 Zitapita izi Yesu anampeza m'Kacisi, nati kwa iye, Taona, waeiritsidwa; usacimwenso, kuti cingakugwere ecipa coposa.
15 Munthuyo anacoka, nauza Ayuda, kuti ndiye Yesu amene adameiritsa.
16 Ndipo cifukwa ca ici Ayuda analondalonda Yesu, popeza anacita izo dzuwa la Sabata.
17 Koma Yesu anayankha iwo, Atate wanga amagwira nchito kufikira tsopano, lnenso ndigwira nchito.
18 Cifukwa ca ici Ayuda anaonjeza kufuna kumupha, si cifukwa ca kuswa dzuwa la Sabata kokha, komatu amaehanso Mulungu Atate wace wa iye yekha; nadziyesera wolingana ndi Mulungu.
19 Pamenepo Yesu anayankha nati kwa iwo, Indetu, indetu, ndinena kwa inu, sakhoza Mwana kucita kanthu pa yekha, koma cimene aona Atate acicita, ndico. Pakuti zimene iye azicita, zomwezo Mwananso azicita momwemo.
20 Pakuti Atate akonda Mwana, namuonetsa zonse azicita yekha: ndipo adzamuonetsa nchito zoposa izi, kuti mukazizwe,
21 Pakuti monga Atate aukitsa akufa, nawapatsa moyo, momwemonso Mwanaapatsa moyo iwo amene iye afuna.
22 Pakuti Atate saweruza munthu ali yense, koma anapereka kuweruza konse kwa Mwana;
23 kuti onse akalemekeze Mwana, monga alemekeza Atate. Wosalemekeza Mwana salemekeza Atate amene anamtuma iye.
24 Indetu, indetu, ndinena kwa inu, kuti iye wakumva mau anga, ndi kukhulupirira iye amene anandituma Ine, ali nao moyo wosatha, ndipo salowa m'kuweruza, koma wacokera kuimfa, nalowa m'moyo.
25 Indetu, indetu, ndinena kwa inu, kuti ikudza nthawi, ndipo Iripo tsopano, imene akufa adzamva mau a Mulungu; ndipo iwo akumva adzakhala ndi moyo.
26 Pakuti monga Atate ali ndi moyo mwa iye yekha, momwemonso anapatsa kwa Mwana kukhala ndi moyo mwa iye yekha;
27 ndipo anampatsa iye mphamvu ya kucita mlandu, pakuti ali Mwana wa munthu.
28 Musazizwe ndi ici, kuti ikudza nthawi, imene onse ali m'manda adzamva mau ace,
29 nadzaturukira, amene adacita zabwino, kukuuka kwa moyo; koma amene adacita zoipa kukuuka kwa kuweruza.
30 Sindikhoza kucita kanthu kwa Ine ndekha; monga momwe ndimva ndiweruza; ndipo maweruzidwe anga ali olungama; cifukwa kuti sinditsata cifuniro canga, koma cifuniro ca Iye ondituma Ine.
31 Ngati ndicita umboni wa Ine ndekha, umboni wanga suli woona.
32 Wocita umboni wa Ine ndi wina; ndipo ndidziwa kuti umboni umene iye andicitira Ine uli woona.
33 Inu munatuma kwa Yohane, ndipo iye anacitira umboni coonadi.
34 Ndipo Ine sindilandira umboni kwa munthu: koma ndinena izi, kuti inu mukapulumutsidwe.
35 Iyeyo anali nyali yoyaka ndi yowala; ndipo inu munafuna kukondwera m'kuunika kwace kanthawi.
36 Koma Ine ndiri nao umboni woposa wa Yohane; pakuti nchito zimene Atateanandipatsa ndizitsirize, nchito zomwezo ndizicita zindicitira umboni, kuti Atate anandituma Ine.
37 Ndipo Atate wonditumayo, 1 Iyeyu wandicitira Ine umboni. Simunamva mau ace konse, kapena maonekedwe ace simunaona.
38 Ndipo mulibe mau ace okhala mwa inu; cifukwa kuti amene Iyeyu anatuma, inu simumkhulupirira ameneyo.
39 2 Musanthula m'malembo, popeza muyesa kuti momwemo muli nao moyo wosatha; ndipo akundicitira Ine umboni ndi iwo omwewo;
40 ndipo 3 simufuna kudza kwa Ine, kuti mukhale nao moyo.
41 4 Ulemu sindiulandira kwa anthu.
42 Koma ndikudziwani inu, kuti mulibe cikondiea Mulungu mwa inu nokha.
43 Ndadza Ine m'dzina la Atate wanga, ndipo simundilandira Ine; akadza wina m'dzina lace la iye mwini, iyeyu mudzamlandira.
44 Mungathe inu bwanji kukhulupira, 5 popeza mulandira ulemu wina kwa mnzace ndipo ulemu wakucokera kwa Mulungu yekha simuufuna?
45 Musayesa kuti Ine ndidzakunenezani inu kwa Atate; 6 pali wakukunenezani, ndiye Mose, amene inu mumtama.
46 Pakuti mukadakhulupirira Mose, mukadakhulupirira Ine; 7 pakuti iyeyu analembera za Ine.
47 Koma ngati simukhulupirira malembo a iyeyu, mudzakhulupirira bwanji mau anga?
1 Zitapita izi anacoka Yesu kunka ku tsidya lija la nyanja ya Galileya, ndiyo ya Tiberiya,
2 Ndipo khamu lalikuru la anthu linamtsata iye, cifukwa anaona zizindikilo zimene anacita pa odwala.
3 Koma Yesu anakwera kuphiri, nakhala pansi komweko pamodzi ndi akuphunzira ace.
4 Ndipo Paskha, phwando la Ayuda, anayandikira.
5 Pamenepo Yesu, pokweza maso ace, ndi kuona kuti khamu lalikuru lirinkudza kwa iye, ananena kwa Filipo, Tidzagula kuti mikate kuti adye awa?
6 Koma ananena ici kuti amuyese; pakuti anadziwa yekha cimene adzacita.
7 Filipo anayankha iye, Mikate ya marupiya atheka mazana awiri siikwanira iwo, kuti yense atenge pang'ono.
8 Mmodzi wa akuphunzira ace, Andreya, mbale wace wa Simoni Petro, ananena ndi Iye,
9 Pali mnyamata pano, amene ali nayo mikate isanu yabarele, ndi tinsomba tiwiri; koma nanga izi zifikira bwanji ambiri otere?
10 N ati Yesu, Akhalitseni anthu pansi, Ndipo panali udzu wambiri pamalopo, Pamenepo amunawo anakhala pansi, kuwerenga kwao monga zikwi zisanu.
11 Pomwepo Yesu anatenga mikateyo; ndipo pamene adayamika, anagawira iwo akukhala pansi; momwemonso ndi tinsomba, monga momwe iwo anafuna.
12 Ndipo pamene adakhuta, Iyeananena kwa akuphunzira ace, Sonkhanitsani makombo kuti kasatayike kanthu.
13 Pomwepo anasonkhanitsa, nadzaza mitanga khumi ndi iwiri ndi makombo a mikate isanuyo yabarele, amene anatsalira anadyawo.
14 Cifukwa cace, anthu, poona cizindikilo cimene anacita, ananena, kuti, Ameneyo ndiye mneneri ndithu wakudzayom'dziko lapansi.
15 Pamenepo Yesu, pozindikira kuti alikufuna kudza kudzamgwira iye, kuti amlonge ufumu, anacokanso kunka kuphiri pa yekha.
16 Koma pofika madzulo, akuphunzira ace anatsikira kunyanja;
17 ndipo pamene adalowa m'ngalawa, analikuoloka nyanja kunka ku Kapernao. Ndipo kutada pamenepo, koma Yesu asanadze kwa iwo.
18 Ndipo nyanja inalikuuka cifukwa ca mphepo yaikulu yakuombako.
19 Ndipo parnene adapalasa monga mastadiya makumi awiri ndi asanu kapena makumi atatu, anaona Yesu alikuyenda panyanja, ndi kuyandikira ngalawa; ndipo anacita mantha.
20 Koma iye ananena nao, ndine; musaope.
21 Pamenepo analola kumlandira m'ngalawa; ndipo pomwepo ngalawayo inafika kumtunda kumene analikunkako.
22 M'mawa mwace khamu la anthu limene linaima tsidya lija la nyanja linaona kuti palibe ngalawa yina koma imodzi, ndi kuti Yesu sanalowa pamodzi ndi akuphunzira ace m'ngalawamo, koma akuphunzira ace adacoka pa okha;
23 koma zinacokera ngalawa zina ku Tiberiya, pafupi pa malo pomwe adadyapo mkate m'mene Yesu adayamika;
24 cifukwa cace pamene khamu la anthu linaona kuti palibe Yesu, ndi akuphunzira ace palibe, iwo okha analowa m'ngalawazo nadza ku Kapernao, alikufuna Yesu.
25 Ndipo pamene anampeza iye tsidya lina la nyanja, anati kwa iye, Rabi, munadza kuno liti?
26 Yesu anayankha iwo nati, Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Mundifuna Ine, si cifukwa munaona zizindikilo, koma cifukwa munadya mkate, nimunakhuta.
27 Gwirani nchito si cifukwa ca cakudya cimene citayika koma ca cakudya cimene citsalira ku moyo wosatha, cimene Mwana wa munthu adzakupatsani inu; pakuti ameneyo Atate, ndiye Mulungu, adamlembera cizindikilo.
28 Pamenepo anati kwa iye, Ticite ciani, kuti ticite nchito za Mulungu?
29 Yesu anayankha nati kwa iwo, Nchito ya Mulungu ndi iyi, kuti mukhulupirire iye amene Iyeyo anamtuma.
30 Cifukwa cace anati kwa iye, Ndipo mucita cizindikilo canji, kuti tione ndi kukhulupirira Inu? mucita ciani?
31 Atate athu anadya mana m'cipululu; monga kwalembedwa, Mkate wocokera m'mwamba anawapatsa iwo kudya,
32 Cifukwa cace Yesu anati kwa iwo, Indetu, indetu, ndinena kwa inu, Si Mose amene anakupatsani inu mkate wa Kumwamba; koma Atate wanga akupatsani inu mkate woona wa Kumwamba.
33 Pakuti mkate wa Mulungu ndiye wakutsika kucokera Kumwamba ndi kupatsa moyo kwa dziko lapansi.
34 Pamenepo anati kwa iye, Ambuye, tipatseni ife mkate umene nthawi zonse.
35 Yesu anati kwa iwo, Ine ndine mkate wamoyo; iye amene adza kwa Ine sadzamva njala, ndi iye amene akhulupirira Ine sadzamva ludzu nthawi zonse.
36 Koma ndinati kwa inu, kuti mungakhale mwandiona, simukhulupirira.
37 Cinthu conse cimene anandipatsa Ine Atate cidzadza kwa Ine; ndipo wakudza kwa Ine sindidzamtaya iye kunja.
38 Pakuti ndinatsika Kumwamba, si kuti ndicite cifuniro canga, koma cifuniro ca iye amene anandituma Ine.
39 Koma cifuniro ca Iye amene anandituma Ine ndi ici, kuti za ici conse Iye anandipatsa Ine ndisatayeko kanthu, koma ndiciukitse tsiku lomariza.
40 Pakuti cifuniro ca Atate wanga ndi ici, kuti yense wakuyang'ana Mwana, ndi kukhulupirira iye, akhale nao moyo wosatha; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomariza.
41 Cifukwa cace Ayuda anang'ung'udza za iye, cifukwa anati, Ine ndine mkate wotsika Kumwamba.
42 Ndipo iwo ananena, Si Yesu uyu, mwana wa Yosefe, atate wace ndi amai wace tiwadziwa? Anena bwanji tsopano, kuti, Ndinatsika Kumwamba?
43 Yesu anayankha nati kwa iwo, Musang'ung'udze winandi mnzace.
44 Kulibe mmodzi akhoza kudza kwa Ine koma ngati Atate wondituma Ine amkoka iye; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomariza.
45 Calembedwa mwa aneneri, Ndipo adzakhala onse ophunzitsidwa ndi Mulungu. 1 Yense amene adamva kwa Atate, naphunzira, adza kwa Ine.
46 2 Sikuti munthu wina waona Atate, koma 3 iye amene ali wocokera kwa Mulungu, ameneyo waona Atate.
47 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, 4 iye wokhuluplra ali nao moyo wosatha.
48 5 Ine ndine mkate wamoyo,
49 6 Makolo anu adadya m'cipululu, ndipo adamwalira.
50 7 Mkate wotsika Kumwamba ndi uwu, kuti munthu akadyeko ndi kusamwalira.
51 8 Mkate wamoyo wotsika Kumwamba Ndine amene. Ngati munthu wina akadyako mkate umene, adzakhala ndi moyo kosatha. Inde, ndipo 9 mkate umene ndidzapatsa Ine, ndiwo thupi langa, ukhale moyo wa dziko lapansi.
52 Pamenepo Ayuda anatetana wina ndi mnzace ndi kunena, Akhoza bwanji ameneyu kutipatsa ife kudya thupi lace?
53 Cifukwa cace Yesu anati kwa iwo, Indetu, indetu, ndinenandi inu, 10 Ngati simukudya thupi la Mwana wa munthu ndi kumwa mwazi wace, mulibe moyo mwa inu nokha.
54 11 Iye wakudya thupi langa ndi kumwa mwazi wanga ali nao moyo wosatha; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomariza.
55 Pakuti thupi langa ndi cakudya ndithu, ndi mwazi wanga ndi caku mwa ndithu.
56 Iye wakudya thupi langa indi kumwa mwazi wanga 12 akhala mwa Ine ndi Ine mwa iye.
57 Monga Atate wamoyo anandituma Ine, ndipo Inenso ndiri ndi moyo cifukwa ca Atate; momwemo wondidya Ine, iyeyu adzakhala ndi moyo cifukwa ca Ine.
58 13 Mkate wotsika Kumwamba ndi umenewu: si monga makolowo, anadya namwalira; iye wakudya mkate umene adzakhala ndi moyo nthawi zonse.
59 Izi ananena m'sunagoge, pakuphunzitsa m'Kapernao.
60 14 Pamenepo ambiri a akuphunzira ace, pakumva izi, anati, Mau awa ndi osautsa; akhoza kumva awa ndani?
61 Koma Yesu podziwa mwa yekha kuti akuphunzira ace alikung'ung'udza cifukwa ca ici, anati kwa iwo, ici mukhumudwa naco?
62 15 Nanga bwanji ngati mukaona Mwana wa munthu alikukwera kumene anali kale lomwe?
63 16 Wopatsa moyo ndi mzimu; thupi silithandiza konse. Mau amene ndalankhula ndi inu ndiwo mzimu, ndi moyo.
64 Koma 17 pali ena mwa inu amene sakhuluplra, Pakuti. Yesu anadziwa poyamba amene ali osakhulupira, ndi amene adzampereka.
65 Ndipo ananena, 18 Cifukwa ca ici ndinati kwa inu, kuti palibe munthu angathe kudza kwa Ine, koma ngati kupatsidwa kwa Iye ndi Atate.
66 19 Pa ici ambiri a akuphunzira ace anabwerera m'mbuyo, ndipo sanayenda-yendanso ndi iye.
67 Cifukwa cace Yesu anati kwa khumi ndi awiriwo, Nanga inunso mufuna kucoka?
68 Simoni Petro anamyankha iye, Ambuye, tidzamuka kwa yani? Inu muli nao mau a moyo wosatha.
69 Ndipo 20 ife tikhulupirira, ndipo tidziwa kuti Inu ndinu Woyera wa Mulungu.
70 Yesu anayankha iwo, 21 Kodi sindinakusankhani khumi ndi awiri, ndipo mwa inu 22 mmodzi ali mdierekezi?
71 Koma adanena za Yudase, mwana wa Simoni Isikariote, pakuti iye ndiye amene akampereka iye, ali mmodzi wa khumi ndi awiri.
1 Ndipo zitapita izi Yesu anayendayenda m'Galileya; pakuti sanafuna kuyendayenda m'Yudeya, cifukwa Ayuda anafuna kumupha iye.
2 Koma phwando la Ayuda, phwando la misasa, linayandikira.
3 Cifukwa cace abale ace anati kwa iye, Cokani pano, mumuke ku Yudeya, kuti akuphunzita anunso akapenye nchito zanu zimenemucita.
4 Pakuti palibe munthu acita kanthu mobisika, nafuna yekha kukhala poyera, Ngati mucita izi, dzionetsereni eni nokha kwa dziko lapansi,
5 Pakuti angakhale abale ace sanakhulupirira iye.
6 Cifukwa cace Yesu ananena nao, Nthawi yanga siinafike; koma nthawi yanu yakonzeka masiku onse.
7 Dziko lapansi silingathe kudana ndi inu; koma Ine lindida popeza Ine ndilicitira umboni, kuti nchito zace ziri zoipa,
8 K werani inu kunka kuphwando; sindikwera Ineku phwando ili tsopano apa; pakuti nthawi yanga siinakwanire.
9 Ndipo m'mene adanena nao zimenezi anakhalabe m'Galileya,
10 Koma pamene abale ace adakwera kunka kuphwando, pomwepo Iyenso anakwera, si poonekera, koma monga mobisalika.
11 Pomwepo Ayuda analikumfuna iye paphwando, nanena, Ali kuti uja?
12 Ndipo kunali kung'ung'udza kwambiri za iye m'makamu a anthu; ena ananena, kuti, Ali wabwino; koma ena ananena, lai, koma asoceretsa khamu la anthuwo.
13 Cinkana anatero panalibe munthu analankhula za iye poyera, cifukwa ca kuopa Ayuda.
14 Koma pamene padafika pakati pa phwando, Yesu anakwera nalowa m'Kacisi, naphunzitsa,
15 Cifukwa cace Ayuda anazizwa, nanena, Ameneyu adziwa bwanji zolemba, wosaphunzira?
16 Pamenepo Yesu anayankha iwo, nati, Ciphunzitso canga siciri canga, koma ca iye amene anandituma Ine.
17 Ngati munthu ali yense afuna kucita cifuniro cace, adzazindikira za ciphunzitsoco, ngati cicokera kwa Mulungu, kapena ndilankhula zocokera kwa Ine ndekha.
18 Iye wolankhula zocokera kwa iye yekha afuna ulemu wa mwini yekha, iye wakufuna ulemu wa iye amene anamtuma, yemweyu ali woona, ndipo mwa iye mulibecosalungama.
19 Si Mose kodi anakupatsani inu cilamulo, ndipo kulibe mmodzi mwa inu acita cilamulo? Mufuna kundipha cifukwa ninji?
20 Khamu la anthu linayankha, Muli ndi ciwanda: afuna ndani kukuphani lou?
21 Yesu anayankha nati kwa iwo, Ndinacita nchito imodzi, ndipo muzizwa monse,
22 Cifukwa ca ici Mose, anakupatsani inu mdulidwe (si kuti ucokera kwa Mose, koma kwa, makolo); ndipo mudula munthu tsiku la Sabata.
23 Ngati munthu alandira mdulidwe tsiku la Sabata, kuti cilamulo ca Mose cingapasulidwe; kodi mundikwiyira Ine, cifukwa ndamciritsadi munthu tsiku la Sabata?
24 Musaweruze monga maonekedwe, koma weruzani ciweruziro colungama.
25 Pamenepo ena a iwo a ku Yerusalemu ananena, Kodi suyu amene afuna kumupha r
26 ndipo taona amalankhula poyera, ndipo sanena kanthu kwa iye. Kapena kodi akuru adziwa ndithu kuti ndiye Kristu ameneyo?
27 Koma ameneyo tidziwa uko acokera: koma Kristu pamene akadzadza, palibe mmodzi adzadziwa uko acokera.
28 Pamenepo Yesu anapfuula m'Kacisi, alikuphunzitsa ndi kunena, Mundidziwa Ine, ndiponso mudziwa uko ndicokera; ndipo sindinadza Ine ndekha, koma iye wondituma Ine amene inu simumdziwa, ali woona.
29 Ine ndimdziwa iye; cifukwa ndiri wocokera kwa iye, nandituma Ine Iyeyu.
30 Pamenepo anafuna kumgwira iye; koma palibe wina anamgwira kumanja, cifukwa nthawi yace siinafike.
31 Koma ambiri a m'khamu la anthu anakhulupirira iye; ndipo ananena, Pamene Kristu akadza kodi adzacita zizindikilo zambiri zoposa zimene adazicita ameneyo?
32 Afarisi anamva khamu la anthu ling'ung'udza zimenezi za iye; ndipo ansembe akulu ndi Afarisi anatuma anyamata kuti akamgwire iye.
33 Pamenepo Yesu anati, Katsala kanthawi ndiri ndi inu, ndipo ndimuka kwa iye wondituma Ine.
34 Mudzafunafuna Ine, osandipeza; ndipo pomwe ndiri Ine, inu simungathe kudzapo.
35 Cifukwa cace Ayuda anati mwa iwo okha, Adzanka kuti uyu kuti ife sitikampeza iye? kodi adzamuka kwa Ahelene obalalikawo, ndi kuphunzitsa Ahelene?
36 Mau awa amene ananena ndi ciani, Mudzandifunafuna osandipeza Ine: ndipo pomwe ndiri Ine, inu simungathe kudzapo?
37 Koma tsiku lomariza, lalikurulo la phwando, Yesu anaimirira napfuula, ndi kunena, Ngati pali munthu akumva Ludzu, adze kwa Ine, namwe.
38 Iye wokhulupirira Ine, monga cilembo cinati, Mitsinje ya madzi amoyo idzayenda, kuturuka m'kati mwace.
39 Koma 1 ici anati za Mzimu, amene iwo akukhulupirira iye anati adzalandire; pakuti Mzimu panalibe pamenepo, cifukwa Yesu sanalemekezedwa panthawi pomwepo.
40 Pamenepo ena a khamulo pakumva mau awa, ananena, 2 Mnene riyo ndi uyu ndithu.
41 Ena ananena, 3 Uyu ndi Kristu, Koma ena ananena, Kodi Kristu adza kuturuka m'Galileya?
42 4 Kodi sicinati cilembo kuti Kristu adza kuturuka mwa mbeu ya Davine, ndi kucokera ku Betelehemu, kumudzi kumene kunali Davine?
43 5 Kudakhala tsono kusiyana m'khamulo cifukwa ca iye.
44 Koma 6 ena mwa iwo anafuna kumgwira iye; koma palibe munthu anamgwira kumanja.
45 Pamenepo anyamatawo anadza kwa ansembe akulu ndi Afarisi; ndipo iwowa anati kwa iwo, Simunamtenga iye bwanji?
46 Anyamatawo anayankha, 7 Nthawi yonse palibe munthu analankhula cotero.
47 Pamenepo Afarisi anayankha iwo, Kodi mwasokeretsedwa inunso?
48 8 Kodi wina wa akuru anakhulupirira iye, kapena wa Afarisi?
49 Koma khamu ili losadziwa cilamulo, likhala lotembereredwa.
50 9 Nikodemo ananena kwa iwo, amene uja adadza kwa iye kale, ali mmodzi wa iwo,
51 Kodi cilamulo cathu ciweruza munthu, osayamba kumva iye, ndi kuzindikira cimene, acita?
52 Anayankha nati kwa iye, Kodi iwenso uli woturuka m'Galileya? Santhula, nuone kuti m'Galileya sanauka mneneri.
53 Ndipo anamuka munthu yense ku nyumba yace.
1 Koma Yesu anamuka ku phiri la Azitona.
2 Komac mamawa anadzanso kuKacisi, ndipo anthu onse anadza kwa iye; ndipo m'mene anakhala pansi anawaphunzitsa.
3 Koma alembi ndi Afarisi anabwera naye kwa iye mkazi wogwidwa m'cigololo, ndipo pamene anamuimika iye pakati,
4 ananena kwa iye, Mphunzitsi, mkazi uyu wagwidwa alimkucita cigololo.
5 Koma m'cilamulo Mose anatilamulira, ttwaponye miyala otere. Cifukwa cace Inu munena ciani za iye?
6 Koma ici ananena kuti amuyese iye, kuti akhale naco comneneza iye. Koma Yesu, m'mene adawerama pansi analemba pansi ndi cala cace.
7 Koma pamene anakhalakhala alikumfunsabe iye, anaweramuka, nati kwa iwo, Amene mwa inu ali wopanda cimo, ayambe kumponya mwala,
8 Ndipo m'mene adaweramanso analemba ndi cala cace pansi.
9 Koma iwo, m'mene adamva, anaturukamo amodzi amodzi, kuyambira akulu, kufikira otsiriza; ndipo Yesu anatsala yekha, ndi mkazi, alikuima pakati.
10 Koma Yesu pamene adaweramuka, anati kwa iye, Mkazi iwe, ali kuti ajawa? Palibe munthu anakutsutsa kodi?
11 Koma iye anati, Palibe, Ambuye. Ndipo Yesu anati, Inenso sindikutsutsa iwe; pita; kuyambira tsopano usacimwenso.
12 Pamenepo Yesu analankhulanso nao, nanena, Ine ndine kuunika kwa dziko lapansi; iye wonditsata ine sadzayenda mumdima, koma adzakhala nako kuunika kwa moyo.
13 Cifukwa cace Afarisi anati kwa iye, Mucita umboni wa Inu nokha; umboni wanu suli woona.
14 Anayankha Yesu nati kwa iwo, Ndingakhale ndicita umboni wa Ine ndekha umboni wanga uli woona; cifukwa ndidziwa kumene ndinacokera ndi kumene ndimukako; koma e inu, simudziwa kumene ndicokera, ndi kumene ndimukako.
15 Inu muweruza monga mwa thupi; Ine sindiweruza munthu.
16 Ndipo ngati ndiweruza Ine, ciweruziro canga ciri coona; pakuti sindiri pa ndekha, koma ine ndi Atate amene anandituma Ine.
17 Inde kudalembedwa m'cilamulo canu kuti umboni wa anthu awiri uli woona.
18 Ine ndine wakucita umboni wa Ine ndekha, ndipo Atate amene anandituma Ine, acita umboni wa Ine.
19 Cifukwa cace ananena ndi iye, Ali kuti Atate, wanu? Yesu anayankha, Simudziwa kapena Ine, kapena Atate wanga; mukadadziwa Ine, mukada-dziwanso Atate wanga.
20 Mau awa analankhula m'nyumba ya cuma ca Mulungu pophunzitsa m'Kacisi; ndipo palibe munthu anamgwira iye, pakuti nthawi yace siinafike.
21 Pamenepo anatinso kwa iwo; Ndimuka Ine, ndipo mudzandifuna, ndipo m'cimo lanu mudzafa: kumene ndimukako Ine, simudziwa kudza inu.
22 Cifukwa cace Ayuda ananena, Kodi adzadzipha yekha, pakuti ananena, Kumene ndimukako Ine, simudziwa inu kudza?
23 Ndipo ananena nao, Inu ndinu ocokera pansi; Ine ndine wocokera Kumwamba; inu ndinu a dziko lino lapansi; sindiri Ine wa dziko lino lapansi.
24 Cifukwa cace ndinati kwa inu, kuti mudzafam'macimo anu, pakuti ngati simukhulupirira kuti Ine ndine, mudzafa m'macimo anu.
25 Pamenepo ananena kwa iye, Ndinu yani? Yesu anati kwa iwo, Cimene comwe ndidalankhulanso ndi inu kuyambira paciyambi.
26 Ndiri nazo zambiri zakulankhula ndi zakuweruza za inu; koma wondituma Ine ali woona; ndipo zimene ndazimva kwa iye, zomwezo ndilankhuia kwa dziko lapansi.
27 Sanazindikira iwo kuti analikunena nao za Atate.
28 Cifukwa cace Yesu anati, Pamene mutadzamkweza Mwana wa munthu, pomwepo mudzazindikira kuti Ine ndine, ndipo sindicita kanthu kwa Ine ndekha, koma monga anandiphunzitsa Atate, ndilankhula izi.
29 Ndipo wondituma Ine ali ndi Ine; sanandisiya Ine pa ndekha; cifukwa ndicita Ine rimene zimkondweretsa iye nthawi zonse.
30 Pakulankhula iye zimenezi, ambiri anakhulupirira iye.
31 Cifukwa cace Yesu ananena kwa Ayuda aja adakhulupirira iye, Ngati mukhala inu m'mau anga, muli akuphunzira anga ndithu;
32 ndipo mudzazindikira coonadi, ndipo coonadi cidzakumasulani.
33 Anamyankha iye, Tiri mbeu ya Abrahamu, ndipo sitinakhala akapolo a munthu nthawi iri yonse; munena bwanji; Mudzayesedwa aufulu?
34 Yesu anayankha iwo, nati, Indetu, indetu, ndinena kwa inu kuti yense wakucita cimo ali kapolo wa cimolo.
35 Koma kapolo sakhala m'nyumba nthawi yonse; mwana ndiye akhala nthawi yonse.
36 Cifukwa cace ngati Mwana adzakuyesani inu aufulu, mudzakhala mfulu ndithu.
37 Ndidziwa kuti muli mbeu ya Abrahamuj koma mufuna kundipha Ine, cifukwa mau anga alibe malo mwa inu.
38 1 Zimene ndinaona Ine kwa Atate, ndilankhula; ndipo inunso mucita cimene mudamva kwa atate wanu.
39 Anayankha nati kwa iye, Atate wathu ndiye Abrahamu. Yesu ananena nao, 2 Ngati muli ana a Abrahamu, mukadacita nchito za Abrahamu.
40 Koma tsopano mufuna kundipha Ine, ndine munthu amene ndinalankhula ndi inu coonadi, 3 cimene ndinamva kwa Mulungu; ici Abrahamu sanacita.
41 Inu mucita nchito za atate wanu. Anati kwa iye, Sitinabadwa ife m'cigololo; tiri naye Atate mmodzi ndiye Mulungu.
42 Yesu anati kwa iwo, 4 Mulungu akadakhala Atate wanu, mukadakonda Ine; pakuti Ine ndinaturuka, ndi kucokera kwa Mulungu; pakuti sindinadza kwa Ine ndekha, koma Iyeyu anandituma Ine.
43 Simuzindikira malankhulidwe anga cifukwa ninji? Cifukwa simungathe kumva mau anga,
44 5 Inu muli ocokera mwa atate wanu mdierekezi, ndipo zolakalaka zace za atate wanu mufuna kucita. Iyeyu anali wambanda kuyambira paciyambi, ndipo sanaima m'coonadi, pakuti mwa iye mulibe coonadi. Pamene alankhula bodza, alankhula za mwini wace; pakuti ali wabodza, ndi atate wace wa bodza.
45 Koma Ine, cifukwa ndinena coonadi, simukhulupirira Ine.
46 Ndani mwa inu anditsutsa Ine za cimo? Ngati ndinena coonadi, simundikhulupirira Ine cifukwa ninji?
47 6 Iye wocokera kwa Mulungu amva zonena za Mulungu; inu simumva cifukwa cakuti simuli a kwa Mulungu,
48 Ayuda anayankha nati kwa iye, Kodi sitinenetsa kun Inu ndinu Msamariya, ndipo 7 muli ndi ciwanda?
49 Yesu anayankha, Ndiribe ciwanda Ine; koma ndilemekeza Atate wanga, ndipo inu mundipeputsa.
50 Koma 8 Ine sinditsata ulemerero wanga; alipo woutsata ndi wakuweruza.
51 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, 9 Munthu akasunga mau anga, sadzaona imfa nthawi yonse.
52 Ayuda anati kwa Iye, Tsopano tazindikira kuti muli ndi ciwanda. 10 Abrahamu anamwalira, ndi aneneri; ndipo Inu munena, Munthu akasunga mau anga, sadzalawa imfa ku nthawi yonse.
53 Kodi Inu ndinu wamkulu ndi atate wathu Abrahamu, amene anamwalira? ndipo aneneri anamwalira: mudziyesera nokha muli yani?
54 Yesu anayankha, Ngati Ine ndidzilemekeza ndekha, ulemerero wanga uli cabe; 11 Atate wanga ndiye wondilemekeza Ine; amene munena za iye, kuti ndiye Mulungu wanu;
55 ndipo 12 inu simunamdziwa iye; koma Ine ndimdziwa iye; ndipo ngati ndinena kuti sindimdziwa iye, ndidzakhala wonama cimodzimodzi inu; koma ndimdziwa iye, ndipo ndisunga mau ace.
56 13 Atate wanu Abrahamu anakondwera kuona tsiku langa; ndipo anaona, nasangalala.
57 Ayuda pamenepo anati kwa iye, Simunafikire zaka makumi asanu, ndipo munaona Abrahamu kodi?
58 Yesu anati kwa iwo, Indetu, indetu, ndinena kwa inu, asanayambe kukhala Abrahamu ndipo 14 Ine ndiripo.
59 Pamenepo 15 anatola miyala kuti amponye iye; koma Yesu anabisala, naturuka m'Kacisi.
1 Ndipo popita, anaona munthu ali wosaona cibadwire.
2 Ndipo akuphunzira ace anamfunsa iye, nanena, Rabi, anacimwa ndani, ameneyo, kapena atate wace ndi amace, kuti anabadwa wosaona?
3 Yesu anayankha, Sanacimwa ameneyo, kapena atate wace ndi amace; koma kuti nchito za Mulungu zikaonetsedwe mwa iye.
4 Tiyenera kugwira nchito za iye wondituma Ine, pokhala pali msana; ukudza usiku pamene palibe munthu angakhoze kugwira nchito,
5 Pakukhala Ine m'dziko lapansi, ndiri kuunika kwa dziko lapansi.
6 Pamene ananena izi, analabvula pansi, nakanda thope ndi malobvuwo, napaka thopelo m'maso,
7 nati kwa iye, Muka, kasambe m'thamanda la Siloamu (ndilolosandulika, Wotumidwa). Pamenepo anacoka, nasamba, nabwera alikuona.
8 Cifukwa cace anzace ndi iwo adamuona kale, kuti anali wopemphapempha, ananena, Kodi si uyu uja wokhala ndi kupemphapempha?
9 Ena ananena, kuti, Ndiyeyu; ena ananena, lai, koma afanana naye. Iyeyu anati, Ndine amene.
10 Pamenepo ananena ndi iye, Nanga maso ako anatseguka bwanji?
11 Iyeyu anayankha, Munthuyo wochedwa Yesu anakanda thope, napaka m'maso mwanga, nati kwa ine, Muka ku Siloamu kasambe; cifukwa cace ndinacoka, ndipo m'mene ndinasamba ndinapenya,
12 Ndipo anati kwa iye, Ali kuti Iyeyo? Anena, Sindidziwa ine.
13 Anapita naye amene anali wosaona kale kwa Afarisi.
14 Koma tsikulo ndi la Sabata limene Yesu anakanda thope, namtsegulira iye maso ace.
15 Pamenepo ndipo Afarisi anamfunsanso, umo anapenyera, Ndipo anati kwa iwo, Anapaka thope m'maso mwanga, ndinasamba, ndipo ndipenya.
16 Ena pamenepo mwa Afarisi ananena, Munthu uyu sacokera kwa Mulungu, cifukwa sasunga Sabata. Koma ena ananena, Munthu ali wocimwa, akhoza bwanji kucita zizindikilo zotere? Ndipo panali kutsutsana mwa iwo.
17 Pamenepo ananenanso kwa wosaonayo, Iwe unenanji za iye, popeza anakutsegulira maso ako? Koma iye anati, Ali Mneneri.
18 Cifukwa cace Ayuda sanakhulupirira za iye, kuti anali wosaona, napenya, kufikira kumene adaitana atate wace ndi amace a iye wopenya;
19 nawafunsa iwo, nanena, Kodi uyu ndi mwana wanu, amene inu munena kuti anabadwa wosaona?
20 Ndipo apenya bwanji tsopano? Atate wace ndi amace anayankha nati, Tidziwa kuti uyu ndi mwana wathu, ndi kuti anabadwa wosaona;
21 koma sitidziwa umo apenyera tsopano; kapena sitimdziwa amene anamtsegulira pamaso pace; mumfunse iye; ali wamsinkhu; adzalankhula mwini za iye yekha.
22 Izi ananena atate wace ndi amace, cifukwa anaopa Ayuda; pakuti Ayuda adapangana kale, kuti ngati munthu ali yense adzambvomereza iye kuti ndiye Kristu, akhale woletsedwa m'sunagoge,
23 Cifukwa ca ici atate wace ndi amace anati, Ali wamsinkhu; mumfunse iye.
24 Pamenepo anamuitana kaciwiri munthuyo amene anali wosaona, nati kwa iye, Lemekeza Mulungu; tidziwa kuti munthuyo ali wocimwa.
25 Pamenepo iyeyu anayankha, Ngati ali wocimwa, sindidziwa; cinthu cimodzi ndicidziwa, pokhala ndinali wosaona, tsopano ndipenya.
26 Cifukwa cace anati kwa iye, Anakucitira iweciani? anakutsegulira iwe maso bwanji?
27 Iye anayankha iwo, Ndinakuuzani kale, ndipo simunamva; mufuna kumvanso bwanji? kodi inunso mufuna kukhala: akuphunzira ace?
28 Ndipo anamlalatira iye, nati, Ndiwe wophunzira wa Iyeyu, ife ndife akuphunzira a Mose.
29 Tidziwa ife kuti Mulungu analankhula ndi Mose; koma sitidziwa kumene acokera ameneyo,
30 Munthuyu anayankha nati kwa iwo, Pakuti cozizwa ciri m'menemo, kuti inu simudziwa kumene acokera, ndipo ananditsegulira maso anga.
31 Tidziwa kuti Mulungu samvera ocimwa. Koma ngati munthu ali yense akhala wopembedza Mulungu nacita cifuniro cace, amvera ameneyo.
32 Kuyambira paciyambi sikunamveka kuti wina anatsegulira maso munthu wosaona cibadwire.
33 Ngatiuyu sanacokera kwa Mulungu, sakadakhoza kucita kanthu.
34 Anayankha natikwa iye, Wabadwa iwe konse m'zoipa, ndipo iwe utiphunzitse ife kodi? Ndipo anamtaya kunja.
35 Yesu anamva kuti adamtaya kunja; ndipo pakumpeza iye, anati, Kodi ukhulupirira Mwana wa Mulungu?
36 Iyeyu anayankha nati, Ndipo ndani iye, Ambuye, kuti ndimkhulupirire iye?
37 Yesu anati kwa iye, Wamuona iye, ndiponso wakulankhula ndi iwe ndi Iyeyo.
38 Koma iye anati, Ndikhulupirira, Ambuye; ndipo anamgwadira iye.
39 Ndipo Yesu anati, Kudzaweruza ndadza Ine ku dziko lino lapansi, kuti iwo osapenya apenye; ndi kuti iwo akupenya akhale osaona,
40 Ndipo Afarisi ena akukhala ndi iye anamva izi, nati kwa iye, Kodi ifenso ndife osaona?
41 Yesu anati kwa iwo, Mukadakhala osaona simukadakhala nalo cimo; koma tsopano munena, kuti, Tipenya: cimo lanu likhala.
1 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Iye wosalowa m'khola la nkhosa pakhomo, koma akwerera kwina, iyeyu ndiye wakuba ndi wolanda.
2 Koma iye wakulowera pakhomo, ndiye mbusa wa nkhosa.
3 Iyeyu, wapakhomo amtsegulira ndi nkhosa zimva mau ace; ndipo aitana nkhosa za iye yekha maina ao, nazitsogolera kunja.
4 Pamene adaturutsa zonse za iye yekha, azitsogolera; ndi nkhosa zimtsata iye; cifukwa zidziwa mau ace.
5 Koma mlendo sizidzamtsata, koma zidzamthawa; cifukwasizidziwa mau a alendo.
6 Fanizo ili Yesu ananena kwa iwo; koma sanazindikira zimene Yesu analikulankhula nao.
7 Cifukwa cace Yesuananenanso nao, Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Ine ndine khomo la nkhosa.
8 Onse amene anadza m'tsogolo mwa Ine ali akuba, ndi olanda: koma nkhosa sizinamva iwo.
9 Ine ndine khomo; ngati wina alowa ndi Ine, adzapulu-mutsidwa, nadzalowa, nadzaturuka, nadzapeza busa.
10 Siikudza mbala, koma kuti ikabe, ndi kupha, ndi kuononga, Ndadza Ine kuti akhale ndi moyo, ndi kukhala nao wocuruka.
11 Ine ndine Mbusa Wabwino; mbusa wabwino ataya moyo wace cifukwa ca nkhosa.
12 Wolipidwa amene sakhala mbusa, amene nkhosa siziri zace za yekha, aona mmbulu ulinkudza, nasiya nkhosazo, nathawa; ndipo mmbulu uzikwatula, nuzibalalitsa;
13 cifukwa ali wolipidwa, ndipo sasamala nkhosa.
14 Ine ndine Mbusa Wabwino; ndipo ndizindikira zanga, ndi zanga zindizindikira ine,
15 monga Atate andidziwa Ine, ndi Ine ndimdziwa Atate; ndipo nditaya moyo wanga cifukwa ca nkhosa.
16 Ndipo nkhosa zina ndiri nazo, zimene siziri za khola ili; izinso ndiyenera kuzitenga, ndipo zidzamva mau anga; ndipo zidzakhala gulu limodzi, mbusa mmodzi,
17 Cifukwa ca ici Atate andikonda Ine, cifukwa nditaya Ine moyo wanga, kuti ndikautengenso,
18 Palibe wina andicotsera uwu, koma ndiutaya Ine ndekha. Ndiri nayo mphamvu yakuutaya, ndi mphamvu ndiri nayo yakuutenganso; lamulo ili ndinalandira kwa. Atate wanga.
19 Panakhalanso kutsutsana pakati pa Ayuda cifukwa ca mau awa.
20 Koma ambiri mwa iwo ananena, Ali ndi ciwanda, nacita misala; mukumva iye bwanji?
21 Ena ananena, Mau awa sali a munthu wogwidwa ciwanda. Kodi ciwanda cikhoza kumtsegulira maso wosaona?
22 Koma kunali phwando la kukonzersanso m'Yerusalemu; nyengoyo ndi yacisanu.
23 Ndipo Yesu analikuyendayenda m'Kacisi m'khumbi la Solomo,
24 Pamenepo Ayuda anamzungulira iye, nanena ndi iye, Kufikira liti musfnkhitsa-slnkhitsa moyo wathu? ngati Inu ndinu Kristu, tiuzeni momveka.
25 Yesu anayankha iwo, Ndakuuzani, ndipo simukhulupirira, Nchitozi ndizicita Ine m'dzina la Atate wanga, zimenezi zindicitira umboni.
26 Koma inu simukhulupira, cifukwa simuli a mwa nkhosa zanga.
27 Nkhosa zanga zimva mau anga, ndipo Ine ndizizindikira, ndipo zinditsata Ine.
28 Ndipo Ine ndizipatsa moyo wosatha; ndipo sizidzaonongeka ku nthawi yonse, ndipo palibe munthu adzazikwatula m'dzanja langa,
29 Atate wanga, amene anandipatsa izo, ali wamkulu ndi onse; ndipo palibe wina angathe kuzikwatula m'dzanja la Atate.
30 Ine ndi Atate ndife amodzi.
31 Ayuda anatolanso miyala kuti amponye iye.
32 Yesu anayankha iwo, ndakuonetsani inu nchito zabwino zambiri za kwa Atate; cifukwa ca nchito yiti ya izo mundiponya miyala?
33 Ayuda anamyankha iye, Cifukwa ca nchito yabwino sitikuponyani miyala, koma cifukwa ca mwano; ndi kuti Inu, muli munthu, mudziyesera nokha Mulungu,
34 Yesu anayankha iwo, Kodi sikulembedwa m'cilamulo canu, Ndinati Ine, Muli milungu?
35 Ngati anawacha milungu iwo amene mau a Mulungu anawadzera (ndipo colemba sicingathe kutyoka),
36 kodi inu munena za iye, amene Atate anampatula namtuma ku dziko lapansi, Ucita mwano; cifukwa ndinati, Ndiri Mwana wa Mulungu?
37 Ngati sindicita nchito za Atate wanga, musakhulupirira Ine.
38 Koma ngati ndicita, mungakhale simukhulupirira Ine, khulupirirani nchitozo; kuti mukadziwe ndi kuzindikira kuti Atate ali mwa Ine, ndi ine mwa Atate.
39 Anafunanso kumgwira iye; ndipo anapulumuka m'dzanja lao.
40 Ndipo anacoka kunkanso tsidya lija la Yordano, kumalo kumene kunali Yohane analikubatiza poyamba paja; ndipo anakhala komweko.
41 Ndipo ambiri anadza kwa iye; nanena kuti, Sanacita cizindikilo Yohane; koma zinthu ziri zonse Yohane ananena za iye zinali zoona.
42 Ndipo ambiri anakhulupirira iye komweko.
1 Koma panali munthu wodwala, Lazaro wa ku Betaniya, wa m'mudzi wa Mariya ndi mbale wace Marita.
2 Koma ndiye Mariya uja anadzoza Ambuye ndi mafuta onunkhira bwino, napukuta mapazi ace ndi tsitsi lace, amene mlongo wace Lazaro anadwala.
3 Pamenepo alongo ace anatumiza kwa iye, nanena, Ambuye, onani, amene mumkonda adwala.
4 Koma Yesu pamene anamva, anati, Kudwala kumene sikuli kwa imfa, koma cifukwa ca ulemerero wa Mulungu, kuti Mwana wa Mulungu alemekezedwe nako.
5 Koma Yesu anakonda Marita, ndi mbale wace, ndi Lazaro.
6 Cifukwa cace pamene anamva kuti anadwala, anakhala pamenepo pa malo pomwepo masiku awiri.
7 Ndipo pambuyo pace ananena kwa akuphunzira ace, Tiyeni tipitenso ku Yudeya.
8 Akuphunzira ananena ndi iye, Ambuye, Ayuda analikufuna kukuponyani miyala tsopano apa; ndipo munkanso komweko kodi?
9 Yesu anayankha, Kodi sikuli maora khumi ndi awiri usana? Ngati munthu ayenda usana sakhumudwa, cifukwa apenya kuunika kwa dziko lino lapansi,
10 Koma ngati munthu ayenda usiku, akhumudwa, cifukwa mulibe kuunika mwa iye.
11 Izi anati, ndipo zitatha izi ananena nao, Lazaro bwenzi lathu ali m'tulo; koma ndimuka kukamuukitsa iye tulo tace.
12 Cifukwa cace akuphunzira ace anati kwa iye, Ambuye, ngati ali m'tulo adzacira.
13 Koma Yesu adanena za imfa yace; koma iwowa anayesa kuti ananena za mpumulo wa tulo.
14 Pamenepo Yesu anati kwa iwo momveka, Lazaro wamwalira.
15 Ndipo ndikondwera cifukwa ca inu kuti kunalibe Ine komweko, cakuti mukakhulupire; koma tiyeni, tipite kwa iye.
16 Pamenepo Tomasi, wochedwa Didimo, anati kwa akuphunzira anzace, Tipite ifenso kuti tikafere naye pamodzi.
17 Ndipo pamene Yesu anadza, anapeza kuti pamenepo atakhala m'manda masiku anai.
18 Koma Betaniya anali pafupi pa Yerusalemu, nthawi yace yonga ya mastadiya khumi ndi asanu;
19 koma ambiri a mwa Ayuda adadza kwa Marita ndi Mariya, kudzawatonthoza mtima pa mlongo wao.
20 Pamenepo Marita, pakumva kuti Yesu alinkudza, anamuka kukakomana ndi iye; koma Mariya anakhalabe m'nyumba.
21 Ndipo Marita anati kwa Yesu, Ambuye, mukadakhala kuno mlongo wanga sakadafa.
22 Koma ngakhale tsopano ndidziwa kuti zinthu ziri zonse mukapempha Mulungu, adzakupatsani Mulungu.
23 Yesu ananena naye, Mlongo wako adzauka.
24 Marita ananena ndi iye, Ndidziwa kuti adzauka m'kuuka tsiku lomariza.
25 Yesu anati kwa iye, Ine ndine kuuka ndi moyo; wokhulupirira Ine, angakhale amwalira, adzakhala ndi moyo;
26 ndipo yense wakukhala ndi moyo, nakhulupirira Ine, sadzamwalira nthawi yonse. Kodi ukhulupirira ici?
27 Ananena ndi iye, Inde Ambuye; ndakhulupirira ine kuti Inu ndinu Kristu, Mwana wa Mulungu, wakudza m'dziko lapansi.
28 Ndipo m'mene anati ici anacoka naitana Mariya mbale wace m'tseri, ndi kuti, Wafika Mphunzitsi, akuitana iwe.
29 Koma iyeyo, pakumva, ananyamuka msanga, nadza kwa iye.
30 (Koma Yesu sanafike kumudzi, koma anali pamalo pomwe Marita adakomana ndi Iye)
31 Pamenepo Ayuda okhala naye m'nyumba, ndi kumtonthoza iye, pakuona Mariya ananyamuka msanga, naturuka, namtsata iye, ndi kuyesa kuti amuka kumanda kukalira komweko.
32 Pomwepo Mariya, pofika pamene panali Yesu, m'mene anamuona iye, anagwa pa mapazi ace, nanena ndi iye, Ambuye, mukadakhala kuno Inu, mlongo wanga sakadamwalira.
33 Pamenepo Yesu, pakumuona iye alikulira, ndi Ayuda akumperekeza iye alikulira, anadzuma mumzimu, nabvutika mwini,
34 nati, Mwamuika iye kuti? Ananena ndi iye, Ambuye, tiyeni, mukaone.
35 Yesu analira.
36 Cifukwa cace Ayuda ananena, Taonani, anamkondadi!
37 Koma ena mwa iwo anati, Kodi uyu wotsegulira maso wosaona uja, sanakhoza kodi kucita kuti sakadafa ameneyunso?
38 Pamenepo Yesu, ndi kudzumanso mwa iye yekha anadza kumanda. Koma panali phanga, ndipo mwala unaikidwa pamenepo.
39 Yesu ananena, Cotsani mwala. Marita, mlongo wace wa womwalirayo, ananena ndi iye, Ambuye, adayamba kununkha: pakuti wagona masiku anai.
40 Yesu ananena naye, Kodi sindinati kwa iwe, kuti, ngati ukhulupira, udzaona ulemerero wa Mulungu?
41 Pomwepo anacotsa mwala. Kama Yesu anakweza maso ace kupenya kumwamba nati, Atate, ndiyamika Inu kuti munamva Ine.
42 Koma ndadziwa Ine kuti mumandimva Ine nthawi zonse; koma cifukwa ca khamu la anthu alikuimirira pozungulira ndinanena ici, kuti akhulupire kuti Inu munandituma Ine.
43 Ndipom'mene adanena izi, ana pfuula ndi mau akuru, Lazaro, turuka.
44 Ndipo womwalirayo anaturuka womangidwa miyendo ndi manja ndi nsaru za kumanda; ndi nkhope yace inazingidwa ndi mlezo. Yesu ananena nao, Mmasuleni iye, ndipo mlekeni amuke.
45 Cifukwa cace ambiri a mwa Ayuda amene anadza kwa Mariya, m'mene anaona cimene anacita, anakhulupirira iye.
46 Koma ena a mwa iwo anamuka kwa Afarisi, nawauza zimene Yesu adazicita.
47 Pamenepo ansembe akulu ndi Afarisi anasonkhanitsa akulu, nanena, Titani ife? cifukwa munthu uyu acita zizindikilo zambiri.
48 Ngati timleka iye kotero, onse adzakhulupirira iye; ndipo adzadza Aroma nadzacotsa malo athu ndi mtundu wathu.
49 Koma wina mmodzi wa mwa iwo, Kayafa, wokhaia mkulu wa ansembe caka comweco anati kwa iwo, Simudziwa kanthu konse inu,
50 kapena simuganiza kuti nkokoma kwa inu kuti munthu mmodzi afere anthu, ndi kuti mtundu wonse usaonongeke,
51 Koma ici sananena kwa iye yekha; koma pokhala mkulu wa ansembe caka comweco ananenera kuti Yesu akadzafera mtunduwo;
52 ndipo si cifukwa ca mtunduwo wokha ai, koma kuti akasonkhanitse pamodzi ana a Mulungu akubalalikawo.
53 Cifukwa cace, kuyambira tsiku Iomwelo anapangana kuti amuphe iye.
54 Cifukwa cace Yesu sanayandeyendanso poonekera mwa Ayuda, koma anacokapo kunka ku dziko loyandikira cipululu, kumudzi dzina lace Efraimu; nakhala komweko pamodzi ndi akuphunzira ace.
55 Koma Paskha wa Ayuda anali pafupi; ndipo ambiri anakwera kunka ku Yerusalemu kucoka ku miraga, usanafike Paskha, kukadziyeretsa iwo okha.
56 Pamenepo analikumfuna Yesu, nanena wina ndi mnzace poimirira iwo m'Kacisi, Muyesa bwanji inu, sadzadza kuphwando kodi?
57 Koma ansembe akulu ndi Afarisi adalamulira, kuti, munthu wina akadziwa pokhala iye, aulule, kuti akamgwire iye.
1 Pomwepo anatsala masiku asanu ndi limodzi asanafike Paskha, Yesu anadza ku Betaniya kumene kunali Lazaro, amene Yesu adamuukitsa kwa akufa.
2 Ndipo anamkonzera iye cakudya komweko; ndipo Marita anatumikira; koma Lazaro anali mmodzi wa iwo akuseama pacakudya pamodzi ndi iye.
3 Pamenepo Mariya m'mene adatenga muyeso umodzi wa mafuta onunkhira bwino a nardo a mtengo wace wapatali, anadzoza mapazi a Yesu, napukuta mapazi ace ndi tsitsi lace; ndipo nyumba inadzazidwa ndi mnunkho wace wa mafutawo.
4 Koma Yudase Isikariote, mmodzi wa akuphunzira ace, amene adzampereka iye, ananena,
5 Nanga mafuta onunkhira awa sanagulitsidwa cifukwa ninji ndi marupiya atheka mazana atatu, ndi kupatsidwa kwa osauka?
6 Koma ananena ici si cifukwa analikusamalira osauka, koma cifukwa anali mbala, ndipo pokhala nalo thumba, amabazoikidwamo.
7 Pamenepo Yesu anati, Mleke iye, pakuti anacisungira ici tsiku la kuikidwa kwanga.
8 Pakuti osauka muli nao pamodzi ndi inu nthawi zonse; koma simuli ndi Ine nthawi zonse.
9 Pamenepo khamu lalikuru la Ayuda Iinadziwa kuti ali pomwepo; ndipo anadza, si cifukwa: ca Yesu yekha, koma kuti adzaone Lazaro, amene adamuukitsa kwa akufa.
10 Koma ansembe akulu anapangana kuti akaphe Lazaronso;
11 pakuti ambiri a Ayuda anacoka cifukwa ca iye, nakhulupirira Yesu.
12 M'mawa mwace khamu lalikuru la anthu amene adadza kuphwando, pakumva kuti Yesu alinkudza ku Yerusalemu,
13 anatenga makwata a kanjedza, naturuka kukakomana ndi iye, napfuula, Hosana; wolemekezeka iye wakudza m'dzina la Ambuye, ndiye Mfumu ya Israyeli.
14 Koma Yesu, m'mene adapeza kaburu anakhala pamenepo; monga mulembedwa:
15 Usaope, mwana wamkazi wa Ziyoni; taona Mfumu yako idza wokhala pa mwana wa buru.
16 Izisanazidziwa aku phunzira ace poyamba; koma pamene Yesu analemekezedwa, pamenepo anakumbukila kuti izi zinalembedwa za iye, ndi kuti adamcitira iye izi.
17 Pamenepo khamulo limene linali pamodzi ndi iye, m'mene anaitana Lazaro kuturuka kumanda, namuukitsa kwa akufa, anacita umboni.
18 Cifukwa ca icinso khamulo linadza kudzakomana ndi iye, cifukwa anamva kuti iye adacita cizindikilo ici.
19 Cifukwa cace Afarisi ananena wina ndi mnzace, Muona kuti simupindula kanthu konse; onani dziko litsata pambuyo pace pa iye.
20 Koma panali Ahelene ena mwa iwo akukwera kunka kukalambira paphwando,
21 Ndipo iwo anadza kwa Filipo wa ku Betsaida wa m'Galileya, namfunsa iye, ndi kuti, Mbuye, tifuna kuona Yesu.
22 Filipo anadza nanena kwa Andreya; nadza Andreya ndi Filipo, nanena ndi Yesu.
23 Koma Yesu anayankha iwo, nati, Yafika nthawi, kuti Mwana wa munthu alemekezedwe.
24 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Ngati mbeu ya tirigu siigwa m'nthaka, nifa, ikhala pa yokha iyo; koma ngati ifa, ibala cipatso cambiri.
25 Iye wokonda moyo wace adzautaya; ndipo wodana ndi moyo wace m'dziko lino lapansi adzausungira ku moyo wosatha.
26 Ngati wina anditumikira Ine, anditsate; ndipo kumene kuli Ine, komwekonso kudzakhala mtumiki wanga, Ngati wina anditumikira Ine, Atate adzamcitira ulemu iyeyu,
27 Moyo wanga wabvutika tsopano; ndipo ndidzanena ciani? Atate, ndipulumutseni Ine ku nthawi iyi. Koma cifukwa ca ici ndinadzera nthawi iyi.
28 Atate, lemekezani dzina lanu. Pomwepo adadza mau ocokera Kumwamba, ndalilemekeza, ndipo ndidzalilemekezanso.
29 Cifukwa cace khamu la anthu akuimirirako, ndi kuwamva ananena kuti kwagunda. Ena ananena, Mngelo walankhula ndi iye.
30 Yesu anayankha nati, Mau awa sanafika cifukwa ca Ine, koma ca inu.
31 Tsopano pali kuweruza kwa dziko ili lapansi; mkulu wa dziko ili lapansi adzatayidwa kunja tsopano,
32 Ndipo Ine, m'mene ndikakwezedwa kudziko, ndidzakoka anthu onse kwa Ine ndekha.
33 Koma ananena ici ndi kuzindikiritsa imfa yanji akuti adzafa nayo.
34 Pamenepo khamulo linayankha iye, Tidamva ife m'cilamulo kuti Kristu akhala ku nthawi yonse; ndipo Inu munena bwanji, kuti Mwana wa munthu ayenera kukwezedwa? Mwana wa munthu amene ndani?
35 Pamenepo Yesu anati kwa iwo, Katsala kanthawi kakang'ono ndipo kuunika kuli mwa inu. 1 Yendani pokhala muli nako kuunika, kuti mdima sungakupezeni; ndipo woyenda mumdima sadziwa kumene amukako,
36 2 Pokhala muli nako kuunika, khulupirirani kuunikako, kuti mukakhale ana a kuunikako. Izi Yesu analankhula, nacoka nawabisalira.
37 Koma angakhale adacita zizindikilo zambiri zotere pamaso pao iwo sanakhulupirira iye;
38 kuti mau a Yesaya mneneri akakwaniridwe, amene anati, 3 Ambuye, wakhulupirira ndani kulalikira kwathu? Ndipo mkono wa Ambuye wabvumbulutsidwa kwa yani?
39 Cifukwa ca ici sanathe kukhulupira, pakuti Yesaya anatinso,
40 4 Wadetsa maso ao, naumitsa mtima wao; Kuti angaone ndi maso, angazindikire ndi mtima, Nangatembenuke, Ndipo ndingawaciritse.
41 5 Izi anati Yesaya, cifukwa anaona ulemerero wace; nalankhula za iye.
42 Kungakhale kotero, ambiri a mwa akuru anakhulupirira iye; koma 6 cifukwa ca Afarisi sanabvomereza, kuti angaletsedwe m'sunagoge,
43 7 pakuti anakonda ulemerero wa anthu koposa ulemerero wa Mulungu.
44 Koma Yesu anapfuula nati, 8 iye wokhulupirira ine, sakhulupirira Ine, koma iye wondituma Ine.
45 Ndipo 9 wondiona Ine aona amene anandituma Ine
46 10 Ndadza Ine kuunika ku dziko lapansi, kuti yense wokhulupirira Ine asakhale mumdima.
47 Ndipo ngati wina akumva mau anga, ndi kusawasunga, Ine sindimweruza; pakuti 11 sindinadza kudzaweruza dziko lapansi, koma kuti ndipulumutse dziko lapansi.
48 12 iye amene akaniza Ine, ndi kusalandira mau anga, ali naye womweruza iye; 13 mau amene ndalankhula, iwowa adzamweruza tsiku lomariza.
49 14 Pakuti sindinalankhula mwa Ine ndekha; koma Atate wondituma Ine, yemweyu anandipatsa Ine lamulo, limene ndikanene, ndi limene ndikalankhule.
50 Ndipo ndidziwa kuti lamulo lace liri moyo wosatha; cifukwa cace zimene ndilankhula, monga momwe Atate wanena ndi Ine, momwemo ndilankhula.
1 Koma pasanafike phwando la Paskha, Yesu, podziwa kuti nthawi yace idadza yakucoka kuturuka m'dziko lino lapansi, kunka kwa Atate, m'mene anakonda ace a iye yekha a m'dziko lapansi, anawakomia kufikira cimariziro.
2 Ndipo pokhala pamgonero, mdierekezi adathakuika mu mtima wace wa Yudase mwana wa Simoni Isikariote, kuti akampereke iye,
3 Yesu, podziwa kuti Atate adampatsa iye zonse m'manja mwace, ndi kuti anacokera kwa Mulungu, namuka kwa Mulungu,
4 ananyamuka pamgonero, nabvula malaya ace; ndipo m'mene adatenga copukutira, anadzimanga m'cuuno.
5 Pomwepo anathira madzi m'nsambidwe, nayamba kusambitsa mapazi a akuphunzira ace, ndi kuwapukuta ndi copukutira, cimene anadzimanga naco,
6 Anadza pomwepo kwa Simoni Petro. Iyeyu ananena ndi iye, Ambuye, kodi Inu mundisambitsa ine mapazi?
7 Yesu anayankha nati kwa iye, Cimene ndicita Ine, sucidziwa tsopano; koma udzadziwa m'tsogolo mwace.
8 Petro ananena ndi iye, Simudzasambitsa mapazi anga ku nthawi yonse. Yesu anamyankha iye, Ngati sindikusambitsa iwe ulibe colandira pamodzi ndi Ine.
9 Simoni Petro ananena ndi iye, Ambuye, si mapazi anga okha, komanse manja ndi mutu.
10 Yesu ananena naye, Amene anatha kusamba alibe kusowa koma kusamba mapazi, koma ayera monse: ndipo inu ndinu oyera, koma si nonse ai.
11 Pakuti anadziwa amene adzampereka iye; cifukwa ca ici anati, Simuli oyera nonse.
12 Pamenepo, atatha iye kusambitsa mapazi ao, ndi kutenga malaya ace, anaseamanso, nati kwa iwo, Nanga cimene ndakucitirani inu; mucizindikira kodi?
13 Inu mundicha Ine Mphunzitsi, ndi Ambuye: ndipo munena bwino; pakuti ndine amene.
14 Cifukwa cace, ngati Ine Ambuye ndi Mphunzitsi, ndasambitsa mapazi anu, inunso muyenera kusambitsana mapazi wina ndi mnzaceo
15 Pakuti ndakupatsani inu citsanzo, kuti, monga Ine ndakucitirani inu, inunso mucite.
16 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Kapolo sali wamkulu ndi mbuye wace; kapena mtumwi sali wamkuru ndi womtuma iye,
17 Ngati mudziwa izi, odala inu ngati muzicita.
18 Sindinena za inu nonse; ndidziwa amene ndawasankha: koma kuti colemba cikwaniridwe, iye wakudya mkate wanga anatsalimira pa Ine cinendene cace.
19 Kuyambira tsopano ndinena kwa inu, cisadacitike, kuti pamene citacitika, mukakhulupire kuti ndine amene.
20 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, Iye wolandira amene ali yense ndimtuma, andilandira Ine; koma wolandira Ine alandira wondituma Ine.
21 Yesu m'mene adanenaizi, anabvutika mumzimu, nacita umboni, nati, Indetu, indetu, ndinena ndi inu, kuti mmodzi wa inu adzandipereka Ine.
22 Akuphunzira analikupenyanawina kwa mnzace, ndi kusinkhasinkha kuti ananena za yani.
23 Koma mmodzi wa akuphunzira ace, amene Yesu anamkonda, analikutsamira pa cifuwa ca Yesu.
24 Pamenepo Simoni Petro anamkodola nanena naye, Utiuze ndiye yani amene anena za iye.
25 Iyeyu potsamira pomwepo, pa cifuwa ca Yesu, anena ndi iye. Ambuye, ndiye yani?
26 Ndipo Yesu anayankha, Ndi iyeyu, amene Ine ndidzamsunsira nthongo ndi kumpatsa, Pamenepo, m'mene anasunsa nthongo anaitenga naipatsa Yudase mwana wa Simoni Isikariote.
27 Ndipopambuyo pace pa nthongoyo, Satana analowa mwa iyeyu. Pamenepo Yesu ananena naye, Cimene ucita, cita msanga,
28 Kama palibe mmodzi wa iwo akuseamako anadziwa cimene anafuna, poti atere naye.
29 Pakuti popeza Yudase anali nalo thumba, enaanalikuyesakuti Yesu ananena kwa iye, Gula zimene zitisowa paphwando; kapena, kuti apatse kanthu kwa aumphawi.
30 Pamenepo iyeyo m'mene adalandira nthongo, anaturuka pomwepo, Koma kunali usiku.
31 Tsono m'mene adaturuka, Yesu ananena, Tsopano walemekezeka Mwana wa munthu, ndipo Mulungu walemekezedwa mwa iye;
32 ndipo Mulungu adzamlemekeza iye mwa iye yekha, adzamlemekeza iye tsopano apa.
33 Tiana, katsala kanthawi ndikhala ndi inu. Mudzandifunafuna Ine; ndipo monga ndinanena kwa Ayuda, kuti kumene ndinkako Ine, inu simungathe kudza, momwemo ndinena kwa inu tsopano.
34 Ndikupatsani inu lamulo latsopano, kuti mukondane wina ndi mnzace; monga ndakonda Inu, kuti inunso mukondane wina ndi mnzace.
35 1 Mwa ici adzazindikira onse kuti muli akuphunzira anga, ngati muli naco cikondano wina ndi mnzace.
36 Simoni Petro anena ndi iye, Ambuye, mumuka kuti? Yesu anayankha, Kumene ndimukako sungathe kunditsata Ine tsopano; koma, 2 udzanditsata bwino lomwe.
37 Petro ananena ndi iye, Ambuye, sindingathe kukutsatani Inu tsopano cifukwa ninji? 3 Ndidzataya moyo wanga cifukwa ca Inu.
38 Yesu anayankha, Moyo wako kodi udzautaya cifukwa ca Ine? Indetu, indetu, ndinena kwa iwe, Asanalire tambala udzandikana Ine katatu.
1 Mtima wanu usabvutike; mukhulupirira Mulungu, khulupirirani Inenso.
2 M'nyumba ya Atate wanga alimo malo okhalamo ambiri. Ngati sikudali kutero, ndikadakuuzani inu; pakuti ndipita kukukonzerani inu malo.
3 Ndipo ngati ndipita kukakonzera inu malo, ndidzabweranso, ndipo ndidzalandira inu kwa Ine ndekha; kuti kumene kuli Ineko, mukakhale inunso.
4 Ndipo kumene ndinkako Ine, mudziwa njira yace.
5 Tomasi ananena ndi Iye, Ambuye, sitidziwa kumene munkako; tidziwa njira bwanji?
6 Yesu ananena naye, ine ndinenjira, ndi coonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine.
7 Mukadazindikira ine mukadadziwa Atate wanganso; kuyambira tsopano mumzindikira iye, ndipo mwamuona iye.
8 Filipo ananena ndi iye, Ambuye, tionetsereni ife Atate, ndipo citikwanira.
9 Yesu ananena naye, Kodi ndiri ndiinu nthawi yaikuru yotere, ndipo sunandizindikira, Filipo? iye amene wandiona Ine waona Atate; unena iwe bwanji, Mutionetsere Atate?
10 Sukhulupirira kodi kuti ndiri Ine mwa Atate, ndi Atate ali mwa Ine? Mau amene ndinena Ine kwa inu sindilankhula kwa Ine ndekha; koma Atate wokhala mwa Ine acita nchito zace.
11 Khulupirirani Ine, kuti Inendiri mwa Atate ndi Atate ali mwa Ine; koma ngati si comweco, khulupirirani Ine cifukwa ca nchito zomwe.
12 Indetu, indetu, ndinena kwa inu, Wokhulupirira Ine, nchito zimene ndicita Ine adzazicitanso iyeyu; ndipo adzacita zoposa izi; cifukwa ndipita Ine kwa Atate.
13 Ndipo cimene ciri conse mukafunse m'dzina langa, ndidzacicita, kuti Atate akalemekezedwe mwa Mwana.
14 Ngati mudzapempha kanthu m'dzina langa, ndidzacita.
15 Ngati mukonda Ine, sungani malamulo anga.
16 Ndipo Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani inu Nkhoswe yina, kuti akhale ndi inu ku nthawi yonse,
17 ndiye Mzimu wa coonadi; amene dziko lapansi silingathe kumlandira, pakuti silimuona iye, kapena kumzindikira iye. Inu mumzindikira iye; cifukwa akhala ndi inu nadzakhala mwa inu.
18 Sindidza-kusiyani inu mukhale ana amasiye; ndidza kwa inu.
19 Katsala kanthawi, ndipo dziko lapansi silindionanso Ine; koma inu mundiona; popeza Ine ndiri ndi moyo inunso mudzakhala ndi moyo.
20 Tsiku lo mwelo mudzazindikira kuti ndiri Ine mwa Atate wanga, ndi inu mwa Ine, ndi Ine mwa inu.
21 Iye wakukhala nao malamulo anga, ndi kuwasunga, iyeyu ndiye wondikonda Ine; koma wondikonda Ine adzakondedwa ndi Atate wanga, ndipo line ndidzamkonda, ndipo ndidzadzionetsandekha kwa iye.
22 Yudase, si Isikariote, ananena ndi iye, Ambuye, cacitika ciani kuti muziti mudzionetsa nokha kwa ife, koma si kwa dziko lapansi?
23 Yesu anayankha nati kwa iye, Ngati wina akonda Ine, adzasunga mau anga; ndipo Atate wanga adzamkonda, ndipo tidzadza kwa iye, ndipo tidzayesa kwa iye mokhalamo.
24 Wosandikonda Ine sasunga mau anga; ndipo 1 mau amene mumva sali mau anga, koma a Atate wondituma Ine.
25 Izi ndalankhula nanu, pakukhala ndi inu.
26 Koma 2 Nkhosweyo, Mzimu Woyera, amene Atate adzamtuma m'dzina langa, 3 Iyeyo adzaphunzitsa Inu zonse, nadzakumbutsa inu zinthu zonse zimene ndinanena kwa inu.
27 4 Mtendere ndikusiyirani inu, mtendere wanga ndikupatsani; Ine sindikupatsani inu monga dziko lapansi lipatsa. 5 Mtima wanu usabvutike, kapena usacite mantha.
28 Mwamva kuti Ine ndinanena kwa inu, 6 Ndimuka, ndipo ndidza kwa inu. Mukadandikonda Ine, mukadakondwera kuti ndipita kwa Atate; 7 pakuti Atate ali wamkuru ndi Ine.
29 Ndipo tsopano 8 ndakuuzani cisanacitike, kuti pamene citacitika mukakhulupire.
30 Sindidzalankhulanso zambiri ndi inu, pakuti 9 mkuru wa dziko lapansi adza; ndipo alibe kanthu mwa Ine;
31 koma kuti dziko lapansi lizindikire kuti ndikonda Atate, ndikuti 10 ndicita monga momwe Atate wandilamulira. Nyamukani, tizimuka kucokera kuno.
1 Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate wanga ndiye wam'munda.
2 Nthambi iri yonse ya mwa Ine yosabala cipatso, aicotsa; ndi iri y'onse yakubala cipatso, aisadza, kuti ikabale cipatso cocuruka.
3 Mwakhala okonzeka tsopano inu cifukwa ca mau amene ndalankhula ndi inu,
4 Khalani mwa Ine, ndi Ine mwa inu. Monga nthambi siingathe kubala cipatso pa yokha, ngati siikhala mwampesa; motere mulibe inunso ngati simukhala mwa Ine.
5 Ine ndine mpesa, inu ndinu nthambi zace: wakukhala mwa Ine, ndi Ine mwa iye, ameneyo abala cipatso cambiri; pakuti kopanda Ine simungathe kucita kanthu.
6 Ngati wina sakhala mwa Ine, watayika kunja monga nthambi, nafota; ndipo azisonkhanitsa nazitaya kumoto, nazitentha.
7 Ngati mukhala mwa Ine, ndi mau anga akhala mwa inu, pemphani cimene ciri conse mucifuna ndipo cidzacitika kwa inu.
8 Mwa ici alemekezedwa Atate wanga, kuti mubale cipatso cambiri; ndipo mudzakhala akuphunzira anga.
9 Monga momwe Atate wandikonda Ine, Inenso ndakonda inu; khalani m'cikondi canga.
10 Ngati musunga malamulo anga mudzakhala m'cikondi canga; monga Ine ndasunga malamulo a Atate wanga, ndipo ndikhala m'cikondi cace.
11 Izi ndalankhula ndi inu, kuti cimwemwe canga cikhale mwa inu, ndi kuti cimwemwe canu cidzale.
12 Lamulo langa ndi ili, kuti mukondane wina ndi mnzace, monga ndakonda inu.
13 Palibe munthu ali naco cikondi coposa ici, cakuti munthu ataya moyo wace cifukwa ca abwenzi ace.
14 Muli abwenzianga inu, ngati muzicita zimene ndikulamulirani inu.
15 Sindichanso inu akapolo; cifukwa kapolo sadziwa cimene mbuye wace acita; koma ndacha inu abwenzi; cifukwa zonse zimene ndazimva kwa Atate wanga ndakudziwitsani.
16 Inu simunandisankha Ine, koma Ine ndinakusankhani inu, ndipo ndinakuikani, kuti mukamuke inu ndi kubala cipatso, ndi kuti cipatso canu cikhale; kuti cimene ciri conse mukapempha Atate m'dzina langa akakupatseni inu.
17 Zinthu izi ndilamulira inu, kuti mukondane wina ndi mnzace.
18 Ngati dziko lapansi lida inu, mudziwa kuti lidada Ine lisanayambe kuda inu.
19 Mukadakhala a dziko lapansi, dziko lapansi likadakonda zace za lokha; koma popeza simuli a dziko lapansi, koma Ine ndinakusankhani inu mwa dziko lapansi, cifukwa ca ici likudani inu.
20 Kumbukilani mau amene Ine ndinanena kwa inu, Kapolo sali wamkuru ndi mbuye wace. Ngati anandilondalonda Ine, adzakulonda-londani inunso; ngati anasunga mau anga, adzasunga anunso.
21 Koma izi zonse adzakucitirani cifukwa ca dzina langa, cifukwa sadziwa wondituma Ine.
22 Sindikadadza ndi kulankhula nao sakadakhala nalo cimo; koma tsopano alibe cowiringula pa macimo ao.
23 Iye wondida Ine, adanso Atate wanga.
24 Sindikadacita mwa iwo nchito zosacita wina, sakadakhala nalo cimo; koma tsopano anaona, nada: Ine ndi Atate wanganso,
25 Koma citero, kuti mau olembedwa m'cilamulo cao akwaniridwe, kuti, Anandida Ine kopanda cifukwa.
26 Koma pamene wafika Nkhoswe, amene Ine ndidzamtuma kwa inu kucokera kwa Atate, ndiye Mzimu wa coonadi, amene aturuka kwa Atate, Iyeyu adzandicitira Ine umboni.
27 Ndipo inunso mucita umboni, pakuti muli ndi Ine kuyambira ciyambi.
1 Izi ndalankhula ndi inu kuti mungakhumudwitsidwe.
2 Adzakuturutsani m'masunagoge; koma ikudza nthawi imene yense wakupha inu adzayesa kuti atumikira Mulungu,
3 Ndipo izi adzacita, cifukwa sanadziwa Atate, kapena Ine.
4 Koma zinthu izi ndalankhula ndi inu kuti ikadza nthawi yao, mukakumbukire kuti ndinakuuzani. Koma izi sindinanena kwa inu kuyambira paciyambi, cifukwa ndinali pamodzi ndi inu.
5 Koma tsopano ndimuka kwa iye wondituma Ine; ndipo palibe wina mwa inu andifunsa Ine, Munka kuti?
6 Koma cifukwa ndalankhula izi ndi inu cisoni cadzala mumtima mwanu.
7 Koma ndinena Ine coonadi ndi inu; kuyenera kwa inu kuti ndicoke Ine; pakuti ngati sindicoka, Nkhosweyo sadzadza kwa inu; koma ngati ndipita ndidzamtuma iye kwa inu.
8 Ndipo atadza Iyeyo, adzatsutsa dziko lapansi za macimo, ndi za cilungamo, ndi za ciweruziro;
9 za macimo, cifukwa sakhulupirira Ine;
10 za cilungamo, cifukwa ndinka kwa Atate, ndipo simundionanso;
11 za ciweruziro, cifukwa mkuru wa dziko ili lapansi waweruzidwa.
12 Ndiri nazo zambirinso zakunena kwa inu, koma simungathe kuzisenza tsopano lino.
13 Koma atadza Iyeyo, Mzimu wa coonadi, adzatsogolera inu m'coonadi conse; pakuti sadzalankhula za iye mwini; koma zinthu ziri zonse adzazimva, adzazilankhula; ndipo zinthu zirinkudza adzakulalikirani.
14 Iyeyo adzalemekeza Ine; cifukwa adzatenga za mwa Ine, nadzalalikira kwa inu.
15 Zinthu ziri zonse Atate ali nazo ndi zanga; cifukwa cace ndinati, kuti atenga za mwa Ine, nadzalalikira kwa inu.
16 Katsala kanthawi, ndipo simundionanso Ine, ndipo kanthawinso, ndipo mudzandiona Ine.
17 Mwa akuphunzira ace tsono anati wina ndi mnzace, ici nciani cimene anena ndi ife, Kanthawi ndipo simundiona; ndiponso kanthawi, ndipo mudzandiona; ndipo, cifukwa ndimuka kwa Atate?
18 Cifukwa cace ananena, ici nciani cimene anena, Kanthawi? Sitidziwa cimene alankhula.
19 Yesu anazindikira kuti analikufuna kumfunsa iye, ndipo anati kwa iwo, Kodi mulikufunsana wina ndi mnzace za ici, kuti ndinati, Kanthawi ndipo simundiona Ine, ndiponso kanthawi nimudzandiona Ine?
20 Indetu, indetu, ndinena ndi inu, kuti mudzalira ndi kubuma maliro inu, koma dziko lapansi lidzakondwera; mudzacita cisoni inu, koma cisoni canu cidzasandulika cimwemwe.
21 Mkazi pamene akuti abale ali naco cisoni, cifukwa yafika nthawi yace; koma pamene wabala mwana, sakumbukilanso kusaukako, cifukwa ca cimwemwe kuti wabadwa munthu ku dziko lapansi.
22 Ndipo inu tsono muli naco cisoni tsopano lino, koma ndidzakuonaninso, ndipo mtima wanu udzakondwera, ndipo palibe wina adzacotsa kwa inu cimwemwe canu.
23 Ndipo tsiku limenelo simudzandifunsa kanthu. Indetu, indetu, ndinena kwa inu, Ngati mudzapempha Atate kanthu, adzakupatsani inu m'dzina langa.
24 Kufikira tsopano simunapempha kanthu m'dzina langa; pemphani, ndipo mudzalandira, kuti cimwemwe canu cikwaniridwe.
25 Zinthu izi ndalankhula ndi inu m'mafanizo; ikudza nthawi imene sindidzalankhula ndi inu m'mafanizo, koma ndidzakulalikirani inu momveka za Atate.
26 Tsiku limenelo mudzapempha m'dzina langa; ndipo sindinena kwa inu kuti Ine ndidzafunsira inu kwa Atate;
27 pakuti Atate yekha akonda inu, cifukwa inu mwandikonda Ine, ndi kukhulupirira kuti Ine ndinaturuka kwa Atate.
28 Ndinaturuka mwa Atate, ndipo ndadza ku dziko lapansi: ndilisiyanso dziko lapansi, ndipo ndipita kwa Atate.
29 Akuphunzira ace ananena, Onani, tsopano mulankhula zomveka, ndipo mulibe kunena ciphiphiritso,
30 Tsopano tidziwa kuti mudziwa zonse, ndipo mulibe kusowa kuti wina akafunse Inu; mwa ici tikhulupirira kuti munaturuka kwa Mulungu.
31 Yesu anayankha iwo, Kodi mukhulupirira tsopano?
32 Onani ikudza nthawi, ndipo yafika, imene mudzabalalitsidwa, yense ku zace za yekha, ndipo mudzandisiya Ine pa ndekha. Ndipo sindikhala pa ndekha, cifukwa Atate ali pamodzi ndi Ine,
33 Zinthu izi ndalankhula ndi inu, kuti mwa Ine mukakhale nao mtendere. M'dziko lapansi mudzakhala naco cibvuto, koma limbikani mtima; ndalilaka dziko lapansi Ine.
1 Zinthu izi analankhula Yesu; ndipo m'mene anakweza maso ace Kumwamba, anati, Atate, yafika nthawi; lemekezani Mwana wanu, kuti Mwana wanu akulemekezeoi Inu;
2 monga mwampatsa iye ulamuliro pa thupi liri lonse, kuti onse amene mwampatsa iye, awapatse iwo moyo wosatha.
3 Koma moyo wosatha ndi uwu, kuti akadziwe Inu Mulungu woona yekha, ndi Yesu Kristu amene munamtuma.
4 Ine ndalemekeza Inu pa dziko lapansi, m'mene ndinatsiriza nchito imene munandipatsa ndicite.
5 Ndipo tsopano, Atate Inu, lemekezani Ine ndi Inu nokha ndi ulemerero umene ndinali nao ndi Inu lisanakhale dziko lapansi.
6 Ndalionetsera dzina lanu kwa anthu amene mwandipatsa Ine m'dziko lapansi; anali anu, ndipo mwandipatsa Ine iwo; ndipo adasunga mau anu.
7 Azindikira tsopane kuti zinthu ziri zonse zimene mwandipatsa Ine zicokera kwa Inu;
8 cifukwa mau amene munandipatsa Ine ndinapatsa iwo; ndipo analandira, nazindikira koona kuti ndinaturuka kwa Inu, ndipo anakhulupira kuti Inu munandituma Ine.
9 Ine ndiwapempherera iwo; sindipempherera dziko lapansi, koma iwo amene mwandipatsa Ine,
10 cifukwa ali anu: ndipo zanga zonse ziri zanu, ndi zanu ziri zanga; ndipo ndilemekezedwa mwa iwo.
11 Sindikhalanso m'dziko lapansi, koma iwo ali m'dziko lapansi, ndipo Ine ndidza kwa Inu. Atate. Woyera, sungani awa m'dzina lanu amene mwandipatsa Ine, kuti akhale mmodzi, monga Ife.
12 Pamenendinakhala nao, Ine ndinalikuwasunga iwo m'dzina lanu amene mwandipatsa Ine; ndipo ndinawasunga, ndipo sanatayika mmodzi yense wa iwo, koma mwana wa citayiko, kuti lembo likwaniridwe.
13 Koma tso pane ndidza kwa Inu; ndipo izi ndilankhula m'dziko lapansi, kuti akhale naco cimwemwe canga cokwaniridwa mwa iwo okha.
14 Ine ndawapatsa iwo mau anu; ndipo dziko lapansi linadana nao, cifukwa sakhala a dziko lapansi, monga Ine sindikhala wa dziko lapansi.
15 Sindipempha kuti muwacotse iwo m'dziko lapansi, koma kuti muwasunge iwo kuletsa woipayo.
16 Siali adziko lapansi monga Ine sindiri wa dziko lapansi.
17 Patulani iwo m'coonadi; mau anu ndi coonadi.
18 Monga momwe munandituma Ine ku dziko lapansi, Inenso ndinatuma iwo ku dziko lapansi,
19 Ndipo cifukwa ca iwo Ine ndidzipatula ndekha kuti iwonso akhale opatulidwa m'coonadi.
20 Koma sindipempherera iwo okha, komanso iwo akukhulupirira Ine cifukwa ca mau ao;
21 kuti onse akakhale amodzi, monga Inu Atate mwa Ine, ndi Ine mwa Inu, kuti iwonso akakhale mwa Ife: kuti dziko lapansi likakhulupire kuti Inu munandituma Ine.
22 Ndipo ulemerero umene mwandipatsa Ine ndapatsa Iwo; kuti akhale amodzi, monga Ife tiri mmodzi;
23 Ine mwa iwo, ndi Inu mwa Ine, kuti akhale angwiro mwa mmodzi; kutr dziko lapansi lizindikire kuti Inu munandituma Ine, nimunawakonda iwo, monga momwe munakonda Ine,
24 1 Atate, amene mwandipatsa Ine, ndifuna kuti, kumene ndiri Ine, iwonso akhale pamodzi ndi Ine; kuti ayang'anire ulemerero wanga, umene mwandipatsa Ine; 2 pakuti munandikonda Inelisanakhazildke dziko lapansi.
25 Atate wolungama, 3 dziko lapansi silinadziwa Inu, koma 4 Ine ndinadziwa Inu; ndipo 5 iwo anazindikira kuti munandituma Ine;
26 ndipo 6 ndinazindikiritsa iwo dzina lanu, ndipo ndidzalizindikiritsa; kuti cikondi 7 cimene munandikonda naco cikhale mwa iwo, ndi Ine mwa iwo.
1 M'mene Yesu adanena izi, anaturuka ndi akuphunzira ace, kunka tsidya lija la mtsinje wa Kedroni, kumene kunali munda, umene analowamo iye ndi akuphunzira ace.
2 Koma Yudasenso amene akampereka iye, anadziwa malowa; cifukwa Yesu akamkako kawiri kawiri ndi akuphunzira ace.
3 Pamenepo Yudase, m'mene adatenga gulu la asilikari ndi anyamata, kwa ansembe akulu ndi Afarisi, anadza komweko ndi nyali ndi miuni ndi zida.
4 Pamenepo Yesu, podziwa zonse zirinkudza pa iye, anaturuka, nati kwa iwo, Mufuna yani?
5 Anayankha iye, Yesu Mnazarayo. Yesu ananena nao, Ndine. Koma Yudase yemwe, wompereka iye, anaima nao pamodzi.
6 Ndipo m'mene anati kwa iwo, Ndine, anabwerera m'mbuyo, nagwa pansi.
7 Pamenepo anawafunsanso, Mufuna yani? koma iwo anati, Yesu Mnazarayo.
8 Yesu anayankha, Ndati, Ndine; cifukwa cace ngati mufuna Ine, lekani awa amuke;
9 kuti akwaniridwe mau amene ati, Mwa iwo amene mwandipatsa Ine, sindinataya mmodzi.
10 Pamenepo Simoni Petro pokhala nalo lupanga, analisolola nakantha kapolo wa mkulu wa ansembe, namsenga khutu lace lamanja. Koma dzina lace la kapoloyo ndiye Malko.
11 Pamenepo Yesu anati kwa Petro, Longa Iupanga m'cimakecace; cikho cimene Atate wandipatsa Ine sindimwere ici kodi?
12 Ndipo khamulo ndi kapitao wamkuru, ndi anyamata a Ayuda anagwira Yesu nammanga iye,
13 nayamba kupita naye kwa Anasi; pakuti anali mpongozi wa Kayafa, amene anali mkulu wa ansembe caka comweco.
14 Koma Kayafa anali uja wakulangiza Ayuda, kuti kuyenera munthu mmodzi afere anthu.
15 Koma Simoni Petro ndi wophunzira wina anatsata Yesu. Koma wophunzira ameneyo anali wodziwika kwa mkulu wa ansembe, nalowa pamodzi ndi Yesu, m'bwalo la mkulu wa ansembe;
16 koma Petro anaima kukhomo kunja, Cifukwa cace wophunzira winayo amene anadziwika kwa mkulu wa ansembe, anaturuka nalankhula ndi wapakhomo, nalowetsa Petro.
17 Pamenepo namwali wapakhomoyo ananena kwa Petro, Kodi suli iwenso wa akuphunzira a munthu uyu? Iyeyu ananena, Sindine.
18 Koma akapolo ndi anyamata analikuimirirako, atasonkha mota wamakara; pakuti kunali kuzizira; ndipo analikuotha moto; koma Petronso anali nao alikuimirira ndi kuotha moto.
19 Ndipo mkulu wa ansembe anafunsa Yesu za akuphunzira ace, ndi ciphunzitso cace.
20 Yesu anayankha iye, Ine ndalankhula zomveka kwa dziko lapansi; ndinaphunzitsa Ine nthawi zonse m'sunagoge ndi m'Kacisi, kumene amasonkhana Ayuda onse; ndipo mobisika sindinalankhula kanthu.
21 Undifunsiranji Ine? funsa iwo amene adamva cimene ndinalankhula nao; taona, amenewo adziwa cimene ndinanena Ine.
22 Koma m'mene iye adanena izi, mmodzi wa anyamata akuimirirako anapanda Yesu khofu, ndi kuti, Kodi uyankha mkulu wa ansembe comweco?
23 Yesu anayankha iye, Ngati ndalankhula coipa, cita umboni wa coipaco, koma ngati bwino, undipandiranji?
24 Koma Anasi adamtumiza iye womangidwa kwa Kayafa mkulu wa ansembe.
25 Koma Simoni Petro analikuimirira ndi kuotha moto. Pomwepo anati kwa iye, Suli iwenso wa akuphunzira ace kodi? Iyeyu anakana, nati, Sindine.
26 Mmodzi wa akapolo a mkulu wa ansembe ndiye mbale wace wa uja amene Petro anamdula khutu, ananena, Ine sindinakuona iwe kodi m'munda pamodzi ndi iye?
27 Pamenepo Petro anakananso; ndipo pomwepo analira tambala.
28 Pamenepo anamtenga Yesu kucokera kwa Kayafa kupita ku Pretorio; koma munali mamawa; ndipo iwo sanalowa ku Pretorio, kuti angadetsedwe, koma kuti akadye Paskha.
29 Cifukwa cace Pilato anaturukira kunja kwa iwo, nati, Cifukwa canji mwadza naco ca munthu uyu?
30 Anayankha nati kwa iye, Akadakhala wosacita zoipa uyu sitikadampereka iye kwa inu.
31 Ndipo Pilato anati kwa iwo, Mumtenge iye inu, ndi kumweruza iye monga mwa cilamulo canu. Ayuda anati kwa iye, Tiribe ulamuliro wakupha munthu ali yense;
32 kuti mau a Yesu akwaniridwe, amene ananena akuzindikiritsa imfa imene, akuti adzafa nayo.
33 Cifukwa cace Pilato analowanso m'Pretorio, naitana Yesu, nati kwa iye, Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda kodi?
34 Yesu anayankha, Kodi munena ici mwa inu nokha, kapena ena anakuuzani za Ine?
35 Pilato anayankha, ndiri ine Myuda kodi? Mtundu wako ndi ansembe akulu anakupereka kwa ine; wacita ciani?
36 Yesu anayankha, Ufumu wanga suli wa dziko lino lapansi; ufumu wanga ukadakhala wa dziko lino lapansi, anyamata anga akadalimbika nkhondo, kuti ndisaperekedwe kwa Ayuda; koma tsopano ufumu wanga suli wocokera konkuno.
37 Pamenepo Pilato anati kwa iye, Nanga kodi ndiwe Mfumu? Yesu anayankha, Munena kuti ndine Mfumu. Ndinabadwira ici Ine, ndipo ndinadzera ici kudza ku dziko lapansi, kuti ndikacite umboni ndi coonadi. Yense wakukhala mwa coonadi amva mau anga.
38 Pilato ananena kwa iye, Coonadi nciani? Ndipo pamene adanena ici, anaturukiranso kwa Ayudawo, nanena nao, vine sindipeza konse cifukwa mwa iye.
39 Koma muli nao makhalidwe, akuti ndimamasulira inu mmodzi pa Paskha; kodi mufuna tsono kuti ndimasulire inu Mfumu ya Ayuda?
40 Pomwepo anapfuulanso, nanena, Si uyu, koma Baraba. Koma Baraba anali wacifwamba.
1 Pamenepo tsono Pilato anatenga Yesu, namkwapula.
2 Ndipo asilikari, m'mene analuka korona waminga anambveka pamutu pace, nampfunda iye maraya acibakuwa;
3 nadza kwa iye, nanena, Tikuoneni, Mfumu ya Ayuda! nampanda khofu.
4 Ndipo Pilato anaturukanso kunja, nanena nao, Taonani, ndidza naye kwa inu kunja kuti mudziwe kuti sindipeza mwa iye cifukwa ciri conse.
5 Pamenepo Yesu anaturuka kunja, atabvala korona waminga; ndi maraya acibakuwa, Ndipo ananena nao, Taonani munthuyu!
6 Ndipo pamene ansembe akulu ndi anyamata anamuona iye, anapfuula nanena, Mpacikeni, mpacikeni, Pilato ananena nao, Mtengeni iye inu nimumpaeike; pakuti ine sindipeza cifukwa mwa: iye.
7 Ayuda anamyankha iye, Tiri naco cilamulo ife, ndipo monga mwa cilamuloco ayenera kufa, cifukwa anadziyesera Mwana wa Mulungu.
8 Ndipo pamene Pilato anamva mau awa, anaopa koposa.
9 Ndipo analowanso ku Pretorio, nanena kwa Yesu, Mucoka kuti? koma Yesu sanamyankha kanthu.
10 Cifukwa cace Pilato ananena kwa iye, Simulankhula ndi ine kodi? simudziwa kodi kuti ulamuliro ndiri nao wakukumasulani, ndipo ndiri nao ulamuliro wakukupacikani?
11 Yesu anamyankha iye, Simukadakhala nao ulamuliro uli wonse pa Ine, ngati sukadapatsidwa kwa inu kucokera Kumwamba; cifukwa ca ici iye wondipereka Ine kwa inu ali nalo cimo loposa.
12 Pa ici Pilato anafuna kumasula iye; koma Ayuda anapfuula, ndi kunena, Ngati mumasula ameneyo, simuli bwenzi la Kaisara; yense wodziyesera yekha mfumu atsutsana naye Kaisara.
13 Pamenepo Pilato, m'mene adamva mau awa, anaturuka ndi Yesu, nakhala pansi pa mpando woweruzira kumalo dzina lace; Bwalo lamiyala, koma m'Cihebri, Gabata,
14 Koma linali tsiku lokonza Paskha; panali monga ora lacisanu ndi cimodzi. Ndipo ananena kwa Ayuda, Taonani, Mfumu yanu!
15 Pamenepo anapfuula iwowa, Cotsani, Cotsani, mpacikeni iye! Pilato ananena nao, Ndipacike Mfumu yanu kodi? Ansembe akulu anayankha, Tiribe Mfumu koma Kaisara.
16 Ndipo pamenepo anampereka iye kwa iwo kutiampacike, Pamenepo anatenga Yesu;
17 ndipo anasenza mtanda yekha, naturuka kunka ku malo ochedwa Maloa-bade, amene achedwa m'Cihebri, Golgota:
18 kumene anampacika Iye; ndipo pamodzi ndi iye awiri ena, cakuno ndi cauko, koma Yesu pakati.
19 Koma Pilato analemba lembo, naliika pamtanda. Koma panalembedwa, YESU MNAZARAYO, MFUMU YA AYUDA.
20 Ndipo lembo ilo analiwerenga ambiri a Ayuda; cifukwa malo amene Yesu anapaeikidwapo anali pafupipa mudziwo; ndipo linalembedwa m'Cihebri, ndi m'Ciroma, ndi m'Cihelene.
21 Pamenepo ansembe akulu a Ayuda, ananena kwa Pilato, Musalembe, Mfumu ya Ayuda; koma kuti Iyeyu anati, Ndiri Mfumu ya Ayuda.
22 Pilato anayankha, Cimene ndalemba, ndalemba.
23 Pamenepo asilikari, m'mene adapacika Yesu, anatenga zobvala zace, nadula panai, natenga wina cina, wina cina, ndiponso maraya; koma maraya anaombedwa monsemo kuyambira pamwamba pace, analibe msoko.
24 Cifukwa cace anati wina kwa mnzace, Tisang'ambe awa, koma ticite maere, awa akhale a yani; kuti lembo likwaniridwe limene linena, Anagawana zobvala zanga mwa iwo okha, ndi pa maraya anga anacitira maere. Ndipo asilikari anacita izi.
25 Koma pamtanda wa Yesu anaimirira amace, ndi mbale wa amace, Mariya, mkazi wa Kleopa, ndi Mariya wa Magadala.
26 Pamenepo Yesu pakuona amace, ndi wophunzira amene anamkonda, alikuimirirako, ananena kwa amace, Mkazi, taonani, mwana wanu!
27 Pamene ananena kwa wophunzirayo, Taona, amai wako. Ndipo kuyambira ora lomweli wophunzirayo ananka naye kwao.
28 Citapita ici Yesu, podziwa kuti zonse zidatha pomwepokuti lembo likwaniridwe, ananena, Ndimva ludzu.
29 Kunaikidwako cotengera codzala ndi vinyo wosasa; cifukwa cace anazenenga cinkhupule codzaza ndi vinyo wosasayo pa phesi lahisope, nacifikitsa kukamwa kwace.
30 Pamene Yesu tsono adalandira vinyo wosasayo anati, Kwatha; ndipo anawerama mutu, napereka mzimu.
31 Pomwepo Ayuda, popeza panali tsiku lokonzera, kuti 1 mitembo ingatsale pamtanda tsiku la Sabata, pakuti tsiku lomwelo la Sabata linali lalikuru, anapempha Pilato kuti miyendo yao ityoledwe, ndipo acotsedwe.
32 Cifukwa cace anadza asilikari natyola miyendo ya woyambayo, ndi ya winayo wopacikidwa pamodzi ndi iye;
33 koma pofika kwa Yesu, m'mene anamuona iye, kuti wafa kale, sanatyola miyendo yace;
34 koma mmodzi wa asilikari anamgwaza ndi nthungo m'nthiti yace, ndipo 2 panaturuka pomwepo mwazi ndi madzi.
35 Ndipo 3 iye amene anaona, wacita umboni, ndi umboni wace uti woona; ndipo iyeyu adziwa kuti anena zoona, kuti inunso mukakhulupire.
36 Pakuti izi zinacitika, kuti lembo likwaniridwe, 4 Pfupa la iye silidzatyoledwa.
37 Ndipo linenanso lembo lina, 5 Adzayang'ana pa iye amene anampyoza.
38 6 Citatha ici. Y osefe wa ku Arimateya, ndiye wophunzira wa Yesu, koma mobisika, cifukwa ca kuopa Ayuda, anapempha Pilato kuti akacotse mtembo wa Yesu. Ndipo Pilato analola. Cifukwa cace anadza, nacotsa mtembo wace.
39 Koma anadzanso 7 Nikodemo, amene anadza kwa iye usiku poyamba paja, alikutenga cisanganizo ca mure ndi aloe, monga miyeso zana.
40 Pamenepo anatenga mtembo wa Yesu, nauzenenga ndi nsaru zabafuta pamodzi ndi zonunkhira, monga mwa maikidwe a maliro a Ayuda.
41 Koma kunali munda kumalo kumene anapacikidwako, ndi m'mundamo munali manda atsopano m'mene sanaikidwamo munthu ali yense nthawi zonse.
42 8 Pomwepo ndipo anaika Yesu, cifukwa ca tsiku lokonzera la Ayuda, pakuti mandawo anali pafupi.
1 Koma tsiku loyamba la Sabata anadza Mariya wa Magadala mamawa, kusanayambe kuca, kumanda, napenya mwala wocotsedwa kumanda.
2 Pomwepo anathamanga nadza kwa Simoni Petro ndi kwa wophunzira wina amene Yesu anamkonda, nanena nao, Anacotsa Ambuye kumanda, ndipo sitidziwa kumene anamuika iye.
3 Anaturuka tsono Petro ndi wophunzira winayo, nalinkupita kumanda.
4 Koma anathamanga onse awiri pamodzi; ndipo wophunzira winayo anathamanga naposa Petro, nayamba kufika kumanda;
5 ndipo m'mene anawerama cosuzumira anaona nsaru zabafuta zitakhala, komatu sanalowamo.
6 Pamenepo anadzanso Simoni Petro alikumtsata iye, nalowa m'manda; ndipo anaona nsaru zabafuta zitakhala,
7 ndi mlezo, umene unali pamutu pace, wosakhala pamodzi ndi nsaru zabafuta, koma wopindika padera pamalo pena.
8 Pamenepo tsono analowanso wophunzira winayo, amene anayamba kufika kumanda, ndipo anaona, nakhulupira.
9 Pakuti kufikira pomwepo sanadziwa lembo lakuti ayenera iye kuuka kwa akufa.
10 Cifukwa cace akuphunzirawo anacokanso, kunka kwao.
11 Koma Mariya analikuima kumanda kunja, alikulira. Ndipo m'mene alikulira anawerama cisuzumirire kumanda;
12 ndipo anaona angelo awiri atabvala zoyera, alikukhala mmodzi kumutu, ndi wina kumiyendo, kumene mtembo wa Yesu udagona.
13 Ndipo iwowa ananena kwa iye, Mkazi, uliranji? Ananena nao, Cifukwa anacotsa Ambuye wanga, ndipo sindidziwa kumene anamuika iye.
14 M'mene adanena izi, anaceuka m'mbuy'o, naona Yesu ali ciriri, ndipo sanadziwa kuti ndiye Yesu.
15 Yesu ananena naye, Mkazi, uliranji? ufuna yani? Iyeyu poyesa kuti ndiye wakumunda, ananena ndi iye, Mbuye ngati mwamnyamula iye, ndiuzeni kumene mwamuika iye, ndipo ndidzamcotsa.
16 Yesu ananena naye, Mariya. Iyeyu m'mene anaceuka, ananena ndi iye m'Cihebri, Raboni; cimene cinenedwa, Mphunzitsi.
17 Yesu ananena naye, Usandikhudze, pakuti sindinatha kukwera kwa Atate; koma pita kwa abale anga, ukati kwa iwo, Ndikwera kunka kwa Atate wanga, ndi Atate wanu, ndi Mulungu wanga, ndi Mulungu wanu.
18 Mariya wa Magadala anapita nalalikira kwa akuphunzirawo, kuti, Ndaona Ambuye; ndi kuti ananena izi kwa iye.
19 Pamenepo, pokhala madzulo, tsiku lomwelo, loyamba la Sabata, makomo ali citsekere, kumene anakhala akuphunzira, cifukwa ca kuopa Ayuda, Yesu anadza naimirira pakati pao, nanena nao, Mtendere ukhale ndi inu.
20 Ndipo pamene adanena ici, anaonetsa iwo manja ace ndi nthiti zace. Pamenepo akuphunzira anakondwera pakuona Ambuye.
21 Cifukwa cace Yesu anatinso kwa iwo, Mtendere ukhale ndi inu; monga Atate wandituma Ine, Inenso ndituma inu.
22 Ndipo pamene anati ici anawapumira, nanena nao, Landirani Mzimu Woyera.
23 Zocimwa za anthu ali onse muwakhululukira, zikhululukidwa kwa iwo; za iwo amene muzigwiritsa, zagwiritsidwa.
24 Koma Tomasi, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, wochedwa Didimo, sanakhala nao pamodzi, pamene Yesu anadza.
25 Cifukwa cace akuphunzira ena ananena naye, Tamuona Ambuye. Koma iye anati kwa iwo, Ndikapanda kuona m'manja ace cizindikilo ca misomaliyo, ndi kuika cala canga m'cizindikilo ca misomaliyo, ndi kuika dzanja langa ku nthiti yace; sindidzakhulupira.
26 Ndipo pakupita masiku asanu ndi atatu akuphunzira ace analinso m'nyumbamo, ndi Tomasi pamodzi nao: Yesu anadza, makomo ali citsekere, naimirira pakati, nati, Mtendere ukhale ndi inu.
27 Pomwepo ananena kwa Tomasi, Bwera naco cala cako kuno, nuone manja anga; ndipo bwera nalo dzanja lako, nuliike ku nthiti yanga, ndipo usakhale wosakhulupira, koma wokhulupira.
28 Tomasi anayankha nati kwa iye, Ambuye wanga, ndi Mulungu wanga.
29 Yesu ananena kwa iye, Cifukwa wandiona Ine, wakhulupira; odala iwo akukhulupira, angakhale sanaona.
30 Ndipo zizindikilo zina zambiri Yesu anazicita pamaso pa akuphunzira ace, zimene sizinalembedwa m'buku ili;
31 koma zalembedwa izi kuti mukakhulupirire kuti Yesu ndiye Kristu Mwana wa Mulungu, ndi kuti pakukhulupira mukhale nao moyo m'dzina lace.
1 Zitapita izi Yesu anadzionetseranso kwa akuphunzira ace ku nyanja ya Tiberiya. Koma anadzionetsera cotere.
2 Anali pamodzi Simoni Petro, ndi Tomasi, wochedwa Didimo, ndi Natanayeli wa ku Kana wa ku Galileya, ndi ana a Zebedayo, ndi awiri ena a akuphunzira ace.
3 Simoni Petro ananena nao, ndinka kukasodza. Ananena naye, Ifenso tipita nawe. Anaturuka, nalowa m'ngalawa; ndipo m'usiku muja sanagwira kanthu.
4 Koma pakuyamba kuca, Yesu anaimirira pam bali pa nyanja, komatu akuphunzirawo sanadziwa kuti ndiye Yesu.
5 Yesu ananena nao, Ananu, muli nako kanthu kakudya kodi? Anamyankha iye, lai.
6 Koma anati kwa iwo, Ponyani khoka ku mbali ya dzanja lamanja ya ngalawa, ndipo mudzapeza, Pamenepo anaponya, ndipo analibenso mphamvu yakulikoka cifukwa ca kucuruka nsomba.
7 Pamenepo wophunzira uja amene Yesu anamkonda ananena kwa Petro, Ndiye Ambuye. Simoni Petro pakumva kuti ndiye Ambuye, anadzibveka maraya a pathupi, pakuti anali wamarisece, nadziponya yekha m'nyanja.
8 Koma akuphunzira ena anadza m'kangalawa, pakuti sanali kutali ndi mtunda, koma monga mikono mazana awiri, nakoka khoka la nsombazo.
9 Ndipo pamene anaturukira pamtunda, anapenya moto wamakara pomwepo, ndi kansomba kosanjikikako, ndi mkate.
10 Yesu ananena nao, Tenganiko nsomba zimene mwazigwira tsopano,
11 Cifukwa cace Simoni Petro anakwera m'ngalawa nakokera khoka kumtunda Iodzala ndi nsomba zazikuru, zana limodzi, ndi makumiasanu ndi zitatu; ndipo zingakhale zinacuruka kotere, kokha silinang'ambika.
12 Yesu ananena nao, Idzani mufisule. Koma palibe mmodzi wa akuphunzira anatha kumfunsa iye, Ndinu yani? podziwa kuti ndiye Ambuye.
13 Yesu anadza natenga mkate napatsa Iwo, momwemonso nsomba.
14 Imeneyo ndi nthawi yacitatu yakudzionetsera Yesu kwa akuphunzira ace, m'mene atauka kwa akufa.
15 Ndipo pamene atafisula Yesu ananena kwa Simoni Petro, Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine koposa awa? Ananena ndi iye, Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu. Ananena naye, Dyetsa ana a nkhosa anga.
16 Ananena nayenso kaciwiri, Simoni mwana wa Yona, ukonda Ine kodi? Ananena ndi iye, Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu. Ananena naye, Weta nkhosa zanga.
17 Ananena: naye kacitatu, Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine? Petro anamva cisoni kuti anati kwa iye kacitatu, Kodi undikonda Ine? ndipo anati kwa iye, Ambuye, mudziwa Inu zonse; muzindikira kuti ndikukondani Inu. Yesu ananena naye, Dyetsa nkhosa zanga.
18 Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, pamene unali mnyamata unadzimangira wekha m'cuuno, ndipo unayenda kumene unafuna; koma pamene udzakalamba udzaturutsa manja ako, ndipo adzakumanga wina, nadzakunyamula kumene sufuna.
19 Koma ici ananena ndi kuzindikiritsa imfa imene adzalemekeza nayo Mulungu. Ndipo m'mene ananena ici, anati kwa iye, nditsate Ine,
20 Petro, m'mene anaceuka, anapenya wophunzira amene Yesu anamkonda alikutsata, amenenso anatsamira pacifuwa pace pamgonero, nati, Ambuye, ndani iye wakupereka Inu?
21 Pamenepo Petro pakumuona, ananena kwa Yesu, Ambuye, koma nanga uyu?
22 Yesu ananena naye, Ngati ndifuna uyu akhale kufikira ndidza Ine, kuli ciani ndi iwe? unditsate Ine iwe.
23 Cifukwa cace mau awa anaturuka kufikira kwa abale, kuti wophunzira uyu sadzafa. Koma Yesu sananena kwa iye kuti sadzafa; koma, Ngati ndifuna iye akhale kufikira ndidza, kuli ciani ndi iwe?
24 Yemweyu ndiye wophunzira wakucita umboniza izi, ndipo analembera izi; ndipo tidziwa kuti umboni wace ndi woona.
25 Koma palinso zina zambiri zimene. Yesu anazicita, zoti zikadalembedwa zonse phe, ndilingalira kuti dziko lapansi silikadakhala nao malo a mabuku amene akadalembedwa. Amen.