1 Ha! mudziwo unadzala anthu, ukhalatu pa wokha! Ukunga mkazi wamasiye! Waukuruwo mwa amitundu, kalonga wamkazi m'madera a dziko Wasanduka wolamba!
2 Uliralira usiku; misozi yace iri pa masaya ace; Mwa onse amene anaukonda mulibe mmodzi wakuutonthoza: Mabwenzi ace onse aucitira ziwembu, Asanduka adani ace.
3 Yuda watengedwa ndende cifukwa ca msauko ndi ukapolo waukuru; Akhala mwa amitundu, sapeza popuma; Onse akumlondola anampeza pakati popsinjikiza.
4 M'njira za Ziyoni mulira posoweka akudzera msonkhano; Pa zipata zace zonse papasuka; ansembe ace onse ausa moyo; Anamwali ace asautsidwa; iye mwini namva zowawa.
5 Amaliwongo ace asanduka akuru ace, adani ace napindula; Pakuti Yehova wamsautsa pocuruka zolakwa zace; Ana ace ang'ono alowa m'ndende pamaso pa adani ace.
6 Ulemu wace wonse wamcokera mwana wamkazi wa Ziyoni; Akalonga ace asanduka nswala zosapeza busa, Anayenda opanda mphamvu pamaso pa wompitikitsa.
7 M'masiku a msauko wace ndi kusocera kwace Yerusalemu ukumbukira zokondweretsa zace zonse zacikhalire; Pogwidwa anthu ace ndi mdaniyo popanda wakuupulumutsa, Adaniwo anamuona naseka mwacipongwe mabwinja ace.
8 Yerusalemu wacimwa kwambiri; cifukwa cace wasanduka cinthu conyansa; Onse akuulemekeza aupeputsa, pakuti auona wamarisece; Inde, uusa moyo, nubwerera m'mbuyo.
9 Udio wace unali m'nsaru zace; sunakumbukira citsiriziro cace; Cifukwa cace watsika mozizwitsa; ulibe wakuutonthoza; Taonani Yehova, msauko wanga, pakuti mdaniyo wadzikuzayekha.
10 Amaliwongo atambasulira manja ao pa zokondweretsa zace zonse; Pakuti waona amitundu atalowa m'malo ace opatulika, Amene munalamulira kuti asalowe mumsonkhano mwanu.
11 Anthu ace onse ausa moyo nafunafuna mkate; Ndi zokondweretsa zao agula zakudya kuti atsitsimutse moyo wao; Taonani, Yehova, nimupenye; pakuti ndasanduka wonyansa.
12 Kodi muyesa cimeneci cabe, nonsenu opita panjira? Penyani nimuone, kodi ciripo cisoni cina ngati cangaci amandimvetsa ine, Cimene Yehova wandisautsa naco tsiku la mkwiyo wace waukali?
13 Anatumiza moto wocokera kumwamba kulowa m'mafupa anga, unawagonjetsa; Wachera mapazi anga ukonde, wandibwezera m'mbuyo; Wandipululutsa ndi kundilefula tsiku lonse.
14 Gori la zolakwa zanga lamangidwa ndi dzanja lace; Zalukidwa, zakwera pakhosi panga; iye wakhumudwitsa mphamvuyanga; Ambuye wandipereka m'manja mwao, sindithai kuwalaka.
15 Ambuye wapepula ngwazi zanga zonse pakati panga; Waitanira msonkhano pa ine kuti uphwanye anyamata anga, Ambuye wapondereza namwaliyo, mwana wamkazi wa Ziyoni, monga mopondera mphesa.
16 Cifukwa ca zimenezi ndilira; diso langa, diso langatu likudza madzi: Pakuti wonditonthoza, wotsitsimutsa moyo wanga, anditarikira; Ana anga asungulumwa, pakuti adaniwo apambana.
17 Ziyoni atambasula manja ace, palibe wakumtonthoza; Yehova walamulira kuti omzungulira Yakobo akhale adani ace; Yerusalemu wasanduka cinthu conyansa pakati pao.
18 Yehova ali wolungama; pakuti ndapikisana ndi m'kamwa mwace: Mudtvetu, mitundu ya anthu nonsenu, nimuone cisoni canga; Anamwali ndi anyamata anga atha kulowa m'ndende.
19 Ndinaitanaakundikondawokoma anandinyenga; Ansembe ndi akulu anga anamwalira m'mudzimu, Alikufunafuna zakudya zotsitsimutsa miyoyo yao.
20 Onani, Yehova; pakuti ndabvutika, m'kati mwanga mugwedezeka; Mtima wanga wasanduka mwa ine; pakuti ndapikisana nanu ndithu; Kunjako lupanga limangopha ana; m'nyumba muli imfa.
21 Iwo anamva kuti ndiusa moyo, palibe wonditonthoza; Adani anga onse atha kumva msauko wanga, nakondwera kuti mwatero ndinu; Mudzafikitsa tsiku lija mwalichula, ndipo iwowo adzanga ine.
22 Zoipa zao zonse zidze pamaso panu, Muwacitire monga mwandicitira ine cifukwa ca zolakwa zanga zonse, Pakuti ndiusa moyo kwambiri, ndi kulefuka mtima wanga,
1 Ambuye waphimbatu ndi mtambo mwana wamkazi wa Ziyoni, pomkwiyira! Wagwetsa pansi kucokera kumwamba kukoma kwace kwa Israyeli; Osakumbukira poponda mapazi ace tsiku la mkwiyo wace.
2 Yehova wameza nyumba zonse za Yakobo osazicitira cisoni; Wagumula malinga a mwana wamkazi wa Yuda mwa ukali wace; Wawagwetsera pansi, waipitsa ufumuwo ndi akalonga ace.
3 Pokwiya moopsya walikha nyanga zonse za Israyeli; Wabweza m'mbuyo dzanja lace lamanja pamaso pa adaniwo, Natentha Yakobo ngati moto wamalawi wonyambita mozungulira.
4 Wathifula uta wace ngati mdani, waima ndi dzanja lace lamanja ngati mmaliwongo; Wapha onse okondweretsa maso; Watsanulira ukali wace ngati moto pa hema wa mwana wamkazi wa Ziyoni.
5 Yehova wasanduka mdani, wameza Israyeli; Wameza zinyumba zace zonse, wapasula malinga ace; Nacurukitsira mwana wamkazi wa Yuda maliro ndi cibumo.
6 Wacotsa mwamphamvu dindiro lace ngati la m'munda; Waononga mosonkhanira mwace; Yehova waiwalitsa anthu msonkhano ndi sabata m'Ziyoni; Wanyoza mfumu ndi wansembe mokwiya mwaukali.
7 Ambuye wataya guwa lace la nsembe, malo ace opatulika amnyansira; Wapereka m'manja a adani ace makoma a zinyumba zace; Iwo anaphokosera m'nyumba ya Yehova ngati tsiku la msonkhano.
8 Yehova watsimikiza mtima kupasula linga la mwana wamkazi wa Ziyoni; Watambalika cingwe, osabweza dzanja lace kuti lisaonongepo; Waliritsa chemba ndi linga; zilefuka pamodzi.
9 Zipata zace zalowa pansi; waononga ndi kutyola mipiringidzo yace; Mfumu yace ndi akalonga ace ali pakati pa amitundu akusowa cilamulo; Inde, aneneri ace samalandira masomphenya kwa Yehova.
10 Akulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala pansi natonthola; Aponya pfumbi pa mitu yao, namangirira ciguduli m'cuuno mwao: Anamwali a ku Yerusalemu aweramitsa pansi mitu yao.
11 Maso anga alefuka ndi misozi, m'kati mwanga mugwedezeka; Ciwindi canga cagwa pansi cifukwa ca kupasuka kwa mwana wamkazi wa anthu amtundu wanga; Cifukwa tiana ndi oyamwa akomoka m'makwalala a mudziwu.
12 Amati kwa amao, Tirigu ndi vinyo ali kuti? Pokomoka iwo ngati olasidwa m'makwalala a mudziwu, Potsanulidwa miyoyo yao pa zifuwa za amao.
13 Ndikucitire umboni wotani? ndikuyerekeze ndi ciani, mwana wamkazi wa Yerusalemu? Ndikulinganize ndi ciani kuti ndikutonthoze, namwaliwe, mwana wamkazi wa Ziyoni? Popeza akula ngati nyanja; ndani angakucize?
14 Aneneri ako anakuonera masomphenya acabe ndi opusa; Osaulula mphulupulu yako kuti abweze undende wako, Koma anakuonera manenero acabe ndi opambutsa.
15 Onse opita panjira akuombera manja: Atsonya, napukusira mitu yao pa mwana wamkazi wa Yerusalemu, nati, Kodi uwu ndi mudzi wochedwa wokongola, wangwiro, wokondweretsa dziko lonse?
16 Adani ako onse ayasamira pa iwe, Atsonya nakukuta mano, nati, Taumeza; Ndithu ili ndi tsiku tinaliyembekezalo, talipeza, taliona.
17 Yehova wacita comwe analingalira; Watsiriza mau ace, amene analamulira nthawi yakale; Wagwetsa osacitira cisoni; Wakondweretsa adani pa iwe, Wakweza nyanga ya amaliwongo ako.
18 Mtima wao unapfuula kwa Ambuye, Linga iwe la mwana wamkazi wa Ziyoni, igwe misozi ngati mtsinje usana ndi usiku; Usapume kanthawi, asaleke mwana wa diso lako.
19 Tauka, tapfuula usiku, poyamba kulonda; Tsanulira mtima wako ngati madzi pamaso pa Ambuye; Takwezera maso ako kwa Iye, cifukwa ca moyo wa tiana tako, Timene tilefuka ndi njala pa malekezero a makwalala onse.
20 Onani Yehova, nimupenye, mwacitira ayani ici? Kodi akazi adzadya zipatso zao, kunena ana amene anawaseweza? Kodi wansembe ndi mneneri adzaphedwa m'malo opatulika a Ambuye?
21 Wamng'ono ndi nkhalamba agona pansi m'makwalala; Anamwali ndi anyamata anga agwa ndi lupanga; Munawapha tsiku la mkwiyo wanu, munawagwaza osacitira cisoni.
22 Mwaitana zondiopsya mozungulira ngati tsiku la msonkhano; Panalibe wopulumuka ndi wotsala tsiku la mkwiyo wa Yehova; Omwe ndinawaseweza ndi kuwalera, adaniwo anawatsiriza.
1 Ine ndine munthuyu wakuona msauko ndi ndodo ya ukali wace.
2 Wanditsogolera, nandiyendetsa mumdima, si m'kuunika ai.
3 Zoonadi amandibwezera-bwezera dzanja lace monditsutsa tsiku lonse.
4 Wagugitsa thupi langa ndi khungu langa, natyola mafupa anga.
5 Wandimangira zitando za nkhondo, wandizinga ndi ulembe ndi mabvuto.
6 Wandikhalitsa mumdima ngati akufakale.
7 Wanditsekereza ndi guta, sindingaturuke; walemeretsa unyolo wanga.
8 Inde, popfuula ine ndi kuitana andithandize amakaniza pemphero langa.
9 Watsekereza njira zanga ndi miya la yosema, nakhotetsa mayendedwe anga.
10 Andikhalira cirombo colalira kapena mkango mobisalira.
11 Wapambutsa njira zanga, nanding'amba; nandipululutsa.
12 Wathifula uta wace, nandiyesa polozetsa mubvi.
13 Walowetsa m'imso mwanga mibvi ya m'phodo mwace.
14 Ndasanduka wondiseka mtundu wanga wonse, ndi nyimbo yao tsiku lonse.
15 Wandidzaza ndi zowawa, wandikhutitsa civumulo.
16 Watyolanso mano anga ndi tinsangalabwi, wandikuta ndi phulusa.
17 Watarikitsanso moyo wanga ndi mtendere; ndinaiwala zabwino.
18 Ndipo ndinati, Mphamvu yanga yatha, osayembekezanso kanthu kwa Yehova.
19 Kumbukirani msauko Wanga ndi kusocera kwanga, ndizo civumulo ndi ndulu.
20 Moyo wanga uzikumbukirabe nuwerama mwa ine,
21 Ndiri naco ciyembekezo popeza ndilingalira ici ndiyembekeza kanthu.
22 Cifukwa cakusathedwa ife ndico cifundo ca Yehova, pakuti cisoni cace sicileka;
23 Cioneka catsopano m'mawa ndi m'mawa; mukhulupirika ndithu.
24 Moyo wanga uti, Gawo langa ndiye Yehova; cifukwa cace ndidzakhulupirira.
25 Yehova akhalira wabwino omlindirira, ndi moyo womfunafuna.
26 Nkokoma kuti munthu ayembekeze ndi kulindirira modekha cipulumutso ca Yehova.
27 Nkokoma kuti munthu asenze gori ali wamng'ono.
28 Akhale pa yekha, natonthole, pakuti Mulungu wamsenzetsa ilo.
29 Aike kamwa lace m'pfumbi; kapena ciripo ciyembekezo.
30 Atembenuzire wompanda tsaya lace, adzazidwe ndi citonzo.
31 Pakuti Yehova sadzataya kufikira nthawi zonse,
32 Angakhale aliritsa, koma adzacitira cisoni monga mwa kucuruka kwa zifundo zace.
33 Pakuti samasautsa dala, ngakhale kumvetsa ana a anthu cisoni.
34 Kupondereza andende onse a m'dziko,
35 Kupambutsa ciweruzo ca munthu pamaso pa Wam'mwambamwamba,
36 Kukhotetsa mlandu wa munthu, zonsezi Ambuye sazikonda.
37 Ndani anganene, conena cace ndi kucitikadi, ngati Ambuye salamulira?
38 Kodi m'kamwa mwa Wam'mwambamwamba simuturuka zobvuta ndi zabwino?
39 Kodi munthu wamoyo adandauliranji pokhala m'zocimwa zace?
40 Tisanthule ntiyese njira zathu ntibwerenso kwa Yehova.
41 Titukulire mitima yathu ndi, manja athu omwe kwa Mulungu ali kumwamba.
42 Ife tilakwa ndi kupikisana nanu, ndipo Inu simunatikhululukira.
43 Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola, mwatipha osacitira cisoni.
44 Mwadzikuta ndi mtambo kuti pemphero lathu lisapyolemo.
45 Mwatiika pakati pa amitundu ngati zinyalala ndi za kudzala.
46 Adani athu onse anatiyasamira,
47 Mantha ndi dzenje zitifikira, ndiphokose ndi cionongeko.
48 M'diso mwanga mutsikamitsinje ya madzi cifukwa ca mwana wamkazi wa anthu amtundu wanga woonongedwa,
49 Diso langa lingotsanulira osaleka, osapumula,
50 Kufikira Yehova adzazolika kumwamba ndi kuona;
51 Diso langa limvetsa moyo wanga zowawa cifukwa ca ana akazi onse a m'mudzi mwanga.
52 Ondida opanda cifukwa anandiinga ngati mbalame;
53 Anaononga moyo wanga m'dzenje, naponya mwala pamwambapaine;
54 Madzi anayenda pamwamba pa mutu panga, ndinati, dalikhidwa.
55 Ndinaitana dzina lanu, Yehova, ndiri m'dzenje lapansi;
56 Munamva mau anga; musabise khutu lanu popuma ndi popfuulaine.
57 Munayandikira tsiku la kukuitanani ine; munati, Usaope.
58 Ambuye munanenera moyo wanga mirandu yace; munaombola moyo wanga.
59 Yehova, mwaona coipa anandicitiraco, mundiweruzire;
60 Mwaona kubwezera kwao konse ndi zopangira zao zonse za pa ine.
61 Mwamva citonzo cao, Yehova, ndi zopangira zao zonse za pa ine,
62 Milomo ya akutsutsana nane ndi zolingalira zao za pa ine tsiku lonse.
63 Taonani kukhala ndi kunyamuka kwao; ndine nyimbo yao.
64 Mudzawabwezera cilango, Yehova, monga mwa macitidwe a manja ao;
65 Muphimbe mtima wao ndi kuwatemberera;
66 Mudzawalondola mokwiya ndi kuwaononga pansi pa thambo la Yehova.
1 Ha! golidi wagugadi; golidi woona woposa wasandulika; Miyala ya malo opatulika yakhutulidwa pa malekezero a makwalalaonse.
2 Ana a Ziyoni a mtengo wapatari, olingana ndi golidi woyengetsa, Angoyesedwa ngati mbiya zadothi zozipanga manja a woumba.
3 Angakhale ankhandwe amapatsa bere, nayamwitsa ana ao; Koma mwana wamkazi wa anthu amtundu wanga wasanduka wankhanza, ngati nthiwatiwa za m'cipululu.
4 Lilime la mwana woyamwa limamatira kumalakalaka kwace ndi ludzu; Ana ang'ono apempha mkate koma palibe wakuwanyemera.
5 Omwe anadya zolongosoka angosiyidwa m'makwalala; Omwe analeredwa nabvekedwa mlangali afungatira madzala.
6 Pakuti mphulupulu ya mwana wamkazi wa anthu amtundu wanga, ikula koposa cimo la Sodomu, Umene unapasuka m'kamphindi, anthu osaucitira kanthu.
7 Omveka ace anakonzeka koposa cipale cofewa, nayera koposa mkaka, Matupi ao anafiira koposa timiyala toti pyu; maonekedwe ao ananga a safiro wa mtengo wapatari.
8 Maonekedwe ao ada koposa makala, sazindikirika m'makwalala; Khungu lao limamatira pa mafupa ao, lakhwinyata, lasanduka ngati ndodo.
9 Ophedwa ndi lupanga amva bwino kupambana ophedwa ndi njala; Pakuti amenewa angokwalika napyozedwa, posowa zipatso za m'munda.
10 Manja a akazi acisoni anaphika anaanao; Anali cakudya cao poonongeka mwana wamkazi wa anthu a mtundu wanga.
11 Yehova wakwaniritsa kuzaza kwace, watsanulira ukali wace; Anayatsa moto m'Ziyoni, unanyambita maziko ace,
12 Mafumu a dziko lapansi sanakhulupirira, ngakhale onse okhala kunja kuno, Kuti adani ndi amaliwongo adzalowadi m'zipata za Yerusalemu.
13 Ndico cifukwa ca macimo a aneneri ndi mphulupulu za ansembeace, Amene anakhetsa mwazi wa olungama pakati pace.
14 Asocera m'makwalala ngati akhungu, aipsidwa ndi mwazi; Anthu sangakhudze zobvala zao.
15 Amapfuula kwa iwo, Cokani, osakonzeka inu, cokani, cokani, musakhudze kanthu. Pothawa iwo ndi kusocera, anthu anati mwa amitundu, Sadzagoneranso kuno.
16 Mkwiyo wa Yehova unawalekanitsa, sadzawasamaliranso; Iwo sanalemekeza ansembe, sanakomera mtima akulu.
17 Maso athu athedwa, tikali ndi moyo, poyembekeza thandizo cabe; Kudikira tinadikira mtundu wosatha kupulumutsa.
18 Amalondola mapazi athu, sitingayende m'makwalala athu; Citsiriziro cathu cayandikira, masiku athu akwaniridwa; pakuti citsiriziro cathu cafikadi.
19 Otilondola anaposa ziombankhanga za m'mlengalenga m'liwilo lao, Anatithamangitsa pamapiri natilalira m'cipululu.
20 Wodzozedwa wa Yehova, ndiye mpweya wa m'mphuno mwathu, anagwidwa m'maenje ao; Amene tinanena kuti, Tidzakhala m'mthunzi mwace pakati pa amitundu,
21 Kondwera nusangalale, mwana wamkazi wa Edomu, wokhala m'dzikola Uzi; Cikho cidzapita ngakhale mwa iwenso; udzaledzera ndi kubvulazako.
22 Mphulupulu yako yatha, mwana wamkazi wa Ziyoni, Yehova sadzakutenganso ndende; Koma adzazonda mphulupulu yako, mwana wa mkazi wa Edomu, nadzabvumbulutsa zocimwa zako.
1 Yehova, kumbukirani cotigweraci, Penyani nimuone citonzo cathu.
2 Colowa cathu casanduka ca alendo, Ndi nyumba zathu za acilendo.
3 Ndife amasiye opanda atate, Amai athu akunga akazi amasiye.
4 Tinamwa madzi athu ndi ndalama, Tiona nkhuni zathu pozigula.
5 Otilondola atigwira pakhosi pathu, Tatopa osaona popumira.
6 Tinagwira mwendo Aigupto Ndi Asuri kuti tikhute zakudya.
7 Atate athu anacimwa, kulibe iwo; Ndipo tanyamula mphulupulu zao.
8 Akapolo atilamulira; Palibe wotipulumutsa m'dzanja lao.
9 Timalowa m'zoopsya potenga zakudya zathu, Cifukwa ca lupanga la m'cipululu,
10 Khungu lathu lapserera ngati pamoto Cifukwa ca kuwawa kwa njala.
11 Anaipitsa akazi m'Ziyoni, Ndi anamwali m'midzi ya Yuda.
12 Anawapacika akalonga manja ao; Sanalemekeza nkhope za akulu.
13 Anyamata ananyamula mphero, Ana nakhumudwa posenza nkhuni.
14 Akulu adatha kuzipata, Anyamata naleka nyimbo zao.
15 Cimwemwe ca mtima wathu calekeka, Masewera athu asanduka maliro.
16 Korona wagwa pamutu pathu; Kalanga ife! pakuti tinacimwa.
17 Cifukwa ca ici mtima wathu ufoka, Cifukwa ca izi maso athu acita cimbuuzi;
18 Pa phiri la Ziyoni lopasukalo Ankhandwe ayendapo.
19 Inu, Yehova, mukhala cikhalire, Ndi mpando wanu wacifumu ku mibadwo mibadwo.
20 Bwanji mutiiwala ciiwalire, Ndi kutisiya masiku ambirimbiri;
21 Mutitembenuzire kwa Inu, Yehova, ndipo tidzatembenuzidwadi, Mukonzenso masiku athu ngati kale lija.
22 Koma mwatikaniza konse, Mwatikwiyira kopambana.