1

1 CIMENE cinaliko kuyambira paciyambi, cimene tidacimva, cimene tidaciona m'maso mwathu, cimene tidacipenyerera, ndipo manja athu adacigwira ca Mau a moyo,

2 (ndipo moyowo unaonekera, ndipo tidaona, ndipo ticita umboni, ndipo tikulalikirani moyo wosathawo, umene unali kwa Atate, nuonekera kwa ife);

3 cimene tidaciona, ndipo tidacimva, tikulatikirani inunso, kuti inunso mukayaniane pamodzi ndi ife; ndipo ciyanjano cathu cirinso ndi Atate, ndipo ndi Mwana wace Yesu Kristu;

4 ndipo izi tilemba ife, kuti cimwemwe cathu cikwaniridwe.

5 Ndipo uwu ndi uthenga tidaumva kwa iye, ndipo tiulalikira kwa inu, kuti Mulungu ndiye kuunika, ndipo mwa iye monse mulibe mdima.

6 Tikati kuti tiyanjana ndi Iye, ndipo tiyenda mumdima, tinama, ndipo siticita coonadi;

7 koma ngati tiyenda m'kuunika, mongalye ali m'kuunika, tiyanjana wina ndi mnzace, ndipo mwazi wa Yesu Mwana wace utisambitsa kuticotsera ucimo wonse.

8 Tikati kuti tiribe ucimo, tidzinyenga tokha, ndipo mwa ife mulibe coonadi.

9 Ngati tibvomereza macimo athu, ali wokhulupirika ndi wolungama iye, kuti atikhululukire macimo athu, ndi kutisambitsa kuticotsera cosalungama ciri conse.

10 Tikanena kutisitidacimwa, timuyesa iye wonama, ndipo mau ace sakhala mwa ife.

2

1 Tiana tanga, izi ndikulemberani, kuti musacimwe. Ndipo akacimwa wina, Nkhoswe tiri naye kwa Atate, ndiye Yesu Kristu wolungama;

2 ndipo iye ndiye ciombolo ca macimo athu; koma wosati athu okha, komanso a dziko lonse lapansi.

3 Ndipo umo tizindikira kuti tamzindikira iye, ngati tisunga malamulo ace.

4 Iye wakunena kuti, Ndimdziwa iye, koma wosasunga malamulo ace, ali wabodza, ndipo mwa iye mulibe coonadi;

5 koma iye amene akasunga mau ace, mwa iyeyu zedi cikondi ca Mulungu cathedwa. M'menemo tizindikira kuti tiri mwa iye;

6 iye wakunena kuti akhala mwa Iye, ayeneranso mwini wace kuyenda monga anayenda Iyeyo.

7 Okondedwa, sindikulemberani lamulo latsopano, komatu lamulo lakale limene munali nalo kuyambira pa ciyambi; Lamulo Iakaielo ndilo mau amene mudawamva.

8 Ndikulemberaninso lamulo latsopano, ndico cimene ciri coona mwa iye ndi mwa inu; kuti mdima ulinkupita, ndi kuunika koona kwayamba kuwala,

9 iye amene anena kuti ali m'kuunika, namuda mbale wace, ali mumdima kufikira tsopane lino.

10 Iye amene akonda mbale wace akhala m'kuunika, ndipo mwa iye mulibe cokhumudwitsa.

11 Koma iye wakumuda mbale wace ali mumdima, nayenda mumdima, ndipo sadziwa kumene amukako, pakuti mdima wamdetsa maso ace.

12 Ndikulemberani, tiana, popeza macimo adakhululukidwa kwa inu mwa dzina lace.

13 Ndikulemberani, atate, popeza mwamzindikira iye amene ali kuyambir paciyambi. Ndikulemberani anyamata, popeza mwamlaka woipavo, Ndakulemberani, ana, popeza mwazindikira Atate.

14 Ndakulemberani, atate, popeza mwamzindikira iye amene ali kuyambira paciyambi. Ndakulemberani, anyamata, popeza muti amphamvu, ndi mau a Mulungu akhala mwa inu, ndipo mwamlaka woipayo.

15 Musakonde dziko lapansi, kapena za m'dziko apansi. Ngati wina akonda dziko lapansi, cikondi ca Atate lsiciri mwa iye.

16 Pakuti ciri conse ca m'dziko lapansi, cilakolakoca thupi ndi cilakolako ca maso, matamandidwe a moyo, sizicokera kwa Atate, koma ku dziko lapansi.

17 Ndipo dziko lapansi lipita, ndi cilakolako cace; koma iye amene acita cifuniro ca Mulungu akhala ku nthawi yonse.

18 Ana inu, ndi nthawi yorsirtza iyi; ndipo monga mudamva kuti wokana. Krisru akudza, ngakhale tsopano alipo okana Kristu ambiri; mwa ici tizindikira kuti ndi nthawi yotsirizira iyi.

19 Anaturuka mwa ife, komatu sanali a ife; pakuti akadakhala a ife akadakhalabe ndi ife, koma kudatero 1 kuti aonekere kutr sali onse a ife.

20 Ndipo 2 inu muti nako kudzoza kocokera kwa Woyerayo, ndipo 3 mudziwa zonse.

21 Sindinakulemberam cifukwa simudziwa coonadi, koma cifukwa muddziwa, ndi cifukwa kulibe bodza locokera kwa coonadi.

22 4 Wabodza ndani, koma iye wokanayo kuti Yesu siali Kristu? iye ndiye wokana Kristu, amene akana Atate ndi Mwana.

23 5 Yense wakukana Mwana, alibe Atate; wobvomereza Mwana ali ndi Atatenso.

24 Koma inu, cimene munacimva kuyambira paciyambi cikhale mwa Inu, 6 Ngari cikhala mwa inu cimene mudacimva kuyambira paciyambi, inunso mudzakhalabe mwa Mwana, ndi mwa Atate.

25 Ndipo 7 ili ndi lonjezano iye anatiloniezera ife, ndiwo moyo wosatha.

26 Izi ndakulemberani za iwo akusokeretsa inu.

27 Ndipo inu, 8 kudzoza kumene munalandira kucokera kwa iye, kukhala mwa inu, ndipo simusowa kuti wina akuphunzitseni; koma 9 monga kudzoza kwace kukuphunzitsani za zinthu zonse, ndipo kuli koona, sikuli bodza ai, ndipo monga kudaphunzitsa inu, mukhale mwa iye.

28 Ndipo tsopano, tiana, khalani mwa iye; kuti 10 akaonekere iye tikakhale nako kulimbika mtima, osacita manyazi kwa iye pa kudza kwace.

29 Ngati mudziwa kuti ali wolungama, muzindikira kuti 11 ali yensenso wakucita cilungamo abadwa kucokera mwa iye.

3

1 Taonani, cikondico Atate watipatsa, kuti tichedwe ana a Mulungu; ndipo tiri ife otere. Mwa ici dziko lapansi silizindikira ife, popeza silimzindikira iye.

2 Okondedwa, tsopano riri ana a Mulungu, ndipo sicinaoneke cimene tidzakhala. Tidziwa kuti, pa kuoneka iye, tidzakhala ofanana ndi iye, Pakuti tidzamuona iye monga ali.

3 Ndipo yense wakukhala naco ciyembekezo ici pa iye, adziyeretsa yekha, monga Iyeyu ali Woyera.

4 Yense wakucita cimo acitanso kusayeruzika; ndipo cimo ndilo kusayeruzika.

5 Ndipo mudziwa kuti iyeyu anaonekera kudzacotsa macimo; ndipo mwa Iye mulibe cimo.

6 Yense wakukhala mwa iye sacimwa; yense wakucimwa sanamuona iye, ndipo sanamdziwa iye.

7 Tiana, munthu asasokeretse inu; iye wakucita colungama af wolungama, monga Iyeyu ali wolungama:

8 iye wocita cimo ali wocokera mwa mdierekezi, cifukwa mdierekezi amacimwa kuyambira paciyambi. Kukacita ici Mwana wa Mulungu adaonekera, ndiko kuti akaononge nchito za mdierekezi,

9 Yense wobadwa kucokera mwa Mulungu sacita cimo, cifukwa mbeu yace ikhala mwa iye; ndipo sakhoza kucimwa, popeza wabadwa kucokera mwa Mulungu.

10 M'menemo aoneka ana a Mulungu, ndi ana a mdierekezi: yense wosacita cilungamo siali wocokera mwa Mulungu; ndi iye wosakonda mbale wace.

11 Pakuti uwu ndi uthenga mudaumva kuyambira paciyambi, kuti tikondane wina ndi mnzace:

12 osati monga Kaini anali wocokera mwa woipayo, namupha mbale wace. Ndipo anamupha iye cifukwa ninji? Popeza nchiro zace zinali zoipa, ndi za mbaie wace zolungama.

13 Musazizwe, abale, Jikadana nanu dziko lapansi.

14 Ife tidziwa kuti tacokera kuturuka muimfa kulowa m'moyo, cifukwa tikondana ndi abale iye amene sakonda akhala muimfa.

15 Yense wakudana ndi mbale wace ali wakupha munthu; ndipo mudziwa kun wakupha munthu ali yense alibe moyo wosatha wakukhala mwa iye.

16 Umo tizindikira cikondi, popeza Iyeyu anapereka moyo wace cifukwa ca ife; ndipo ife tiyener kupereka moyo wathu cifukwa ca abale.

17 Koma iye amene ali naco coma ca dziko lapansi, naona mbale wace ali wosowa ndi kutsekereza cifundo cace pommana iye, nanga cikondi ca Mulungu cikhala mwa iye bwanji?

18 Tiana, tisakonde ndi mau, kapena ndi lilime, komatu ndi kucita ndi m'coonadi.

19 Umo tidzazindikira kuti tiri ocokera m'coonadi, ndipo tidzakhazikitsa mtima wathu pamaso pace,

20 1 m'mene monse mtima wathu utitsutsa; cifukwa Mulungu ali wamkuru woposa mitima yathu, nazindikira zonse.

21 Okondedwa, 2 mtima wathu ukapanda kuritsutsa, tiri nako kulimbika mtima mwa Mulungu;

22 ndipo 3 cimene ciri conse tipempha, tilandira kwa iye, cifukwa tisunga malamulo ace, ndipo ticita zomkondweretsa pamaso pace.

23 Ndipo 4 Lamulo lace ndi ili, kuti tikhulupirire dzina la Mwana wace Yesu Kristu, ndi 5 kukondana wina ndi mnzace, monga anatilamulira.

24 Ndipo 6 munthu amene asunga malamulo ace akhala mwa iye, ndi iye mwa munthuyo. Ndipo 7 m'menemo tizindikira kuti akhala mwa ife, kucokera mwa Mzimu amene anatipatsa ife.

4

1 Okondedwa, musamakhulupirira mzimu uli wonse, koma yesani mizimu ngati icokera mwa Mulungu: popeza aneneri onyenga ambiri anaturuka kulowa m'dziko lapansi.

2 M'menemo muzindikira Mzimu Wl Mulungu: mzimu uli wonse umen ubvomereza kuti Yesu Kristu ana dza m'thupi, ucokera mwa. Mulungu

3 ndipo mzimu uli wonse umen subvomereza Yesu sucokera kwa Mulungu; ndipo uwu ndiwo mzirm wa wokana Kristu umene mudamvi kuti ukudza; ndipo ulimo m'dziko lapansi tsopano lomwe,

4 Inu ndinu ocokera mwa Mulungu, tiana, ndipo munailaka; pakuti iye wakukhah mwa inu aposa iye wakukhala m'dzi ko lapansi. Iwo ndiwo ocoken m'dziko lapansi;

5 mwa ici alankhula monga ocokera m'dziko lapansi, ndipo dziko tapansi liwamve ra.

6 Ife ndife ocokera mwa Mu lungu; iye amene azindikira Mu lungu atimvera; iye wosacoken mwa Mulungu satimvera ife. Mo mwemo tizindikira mzimu wa coonadi, ndi mzimu wa cisokeretso.

7 Okondedwa, tikondane wins ndi mnzace: cifukwa kuti cikond cicokera kwa Mulungu, ndipo yense amene akonda, abadwa kucokera kwa Mulungu, namzindikira Mulungu,

8 iye wosakonda sazindikira Mulungu; cifukwa Mulungu ndiye cikondi.

9 Umo cidaoneka cikondi ca Mulungu mwa ife, kuti Mulungu anamtuma Mwana wace wobadwa yekha alowe m'dziko lapansi, kuti tikhale ndi moyo mwa iye.

10 Umo muli cikondi, sikuti ife tinakonda Mulungu, koma kuti iye anatikonda ife, ndipo anatuma Mwana wace akhale ciombolo cifukwa ca macime athu.

11 Okondedwa, ngati Mulungu anatikonda ife kotero, ffenso tiyenera kukondana wina ndi mnzaceo

12 Palibe munthu adamuona Mulungu nthawi iri yonse; tikakondana wina ndi mnzace, Mulungu akhala mwa ife, ndi cikondi cace cikhala cangwiro mwa ife;

13 m'menemo tizindikira kuti tikhala mwa iye, ndi iye mwa ife, cifukwa anatipatsako Mzimu wace.

14 Ndipo ife tapenyera, ndipo ticita umboni kuti Atate anatuma Mwana akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi.

15 Iye amene adzabvomereza kuti Yesu ali Mwana wa Mulungu, Mulungu akhala mwa iye, ndi iye mwa Mulungu.

16 Ndipo ife tazindikira, ndipo takhulupirira cikondico Mulungu ali naco pa ife. Mulungu ndiye cikondi, ndipo iye amene akhala m'cikondi akhala mwa Mulungu, ndipo Mulungu akhala mwa iye.

17 M'menemo cikondi cathu cikhala cangwiro kuti tikhale nako kulimbika mtima m'tsiku la mlandu; citukwa monga Iyeyuali, momwemo tiri ife m'dziko line lapansi.

18 Mulibe mantha m'cikondi; koma cikondi cangwiro citaya kunja mantha, popeza mantha ali naco cilango, ndipo wamanthayo sakhala wangwiro m'cikondi.

19 Tikonda ife, cifukwa anayamba iye kutikonda.

20 Munthu akati, kuti, Ndikonda Mulungu, nadana naye mbale wace, ali wabodza: pakuti iye wosakonda mbale ware amene wamuona, sakhoza kukonda Mulungu amene sanamuona.

21 Ndipo lamulo ili tiri nalo locokera kwa iye, kuti iye amene akonda Mulungu akondenso mbale wace.

5

1 Yense wokhulupirira kuti Yesu ndiye Kristu wabadwa kucokera kwa Mulungu; ndipo yense wakukonda iye amene anabala akondanso iye amene anabadwa wocokera mwa iye.

2 Umo tizindikira kuti tikonda ana a Mulungu, pamene tikonda Mulungu, ndi kucita malamulo ace.

3 Pakuti ici ndi cikondi ca Mulungu, kuti tisunge malamulo ace: ndipo malamulo ace sali olemetsa.

4 Pakuti ciri conse cabadwa mwa Mulungu cililaka dziko lapansi; ndipo ici ndi cilako tililaka naco dziko lapansi, ndico cikhulupiriro cathu.

5 Koma ndani iye wolilaka dziko lapansi, koma iye amene akhulupirira kuti Yesu ndiye Mwana wa Mulungu

6 iye ndiye amene adadza mwa madzi ndi mwazi; ndiye Yesu Kristu; wosati ndi madzi okha, koma ndi madzi ndi mwazi.

7 Ndipo Mzimu ndiye wakucita umboni, cifukwa Mzimu ndiye coonadi,

8 Pakuti pali atatu akucita umboni, Mzimu, ndi madzi, ndi mwazi; ndipo iwo atatu ali mmodzi.

9 Ngati tilandira umboni wa anthu, umboni wa Mulungu uposa; cifukwa umboni wa Mulungu ndi uwu, kuti anacita umboni za Mwana wace.

10 Iye amene amkhulupirira Mwana wa Mulungu ali nao umboni mwa iye; ye wosakhulupirira Mulungu ananuyesa iye wonama; cifukwa sanakhulupirira umboni wa Mulungu anaucita wa Mwana wace.

11 Ndipo uwu ndi umboniwo, kuti Mulungu anatipatsa ife moyo wosatha, ndipo moyo umene uli mwa Mwana wace.

12 Iye wakukhala ndi Mwana ali nao moyo; wosakhala ndi Mwana wa Mulungu alibe moyo.

13 Izi ndakulemberani, kuti mudziwe kuti muli ndi moyo wosatha, inu amene mukhulupirira dzina la Mwana wa Mulungu.

14 Ndipo uku ndi kulimbika mrima kumene tiri nako kwa iye, kuti ngati tipempha kanthu monga mwa cifuniro cace, atimvera;

15 ndipo ngati tidziwa kuti atimvera ciri conse ticipempha, tidziwa kuti tiri nazo izi tazipempha kwa iye.

16 Wina akaona mbale wace alikucimwa cimo losati la kuimfa, apemphere Mulungu, ndipo iye adzampatsira moyo wa iwo akucita macimo osati a kuimfa. Pali cimo la kuimfa: za ililo sindinena kuti mupemphere.

17 Cosalungama ciri conse ciri ucimo; ndipo pali cimo losati la kuimfa.

18 Tidziwa kuti yense wobadwa kucokera mwa Mulungu sacimwa, koma iye wobadwa kucokera mwa Mulungu adzisunga yekha, ndipo woipayo samkhudza.

19 Tidziwa kuti tiri ife ocokera mwa Mulungu, ndipo dziko lonse lapansi ligona mwa woipayo.

20 Ndipo tidziwa kuti Mwana wa Mulungu wafika, natipatsa ife cidziwitso, kuti tizindikire Woonayo, ndipo tiri mwa Woonayo, mwa Mwana wace Yesu Kristu. Iye ndiye Mulungu woona ndi moyo wosatha.

21 Tiana, 1 dzisungireni nokha kupewa mafano.