1 PAULO, mtumwi wa Kristu Yesu mwa cifuniro ca Mulungu, ndi Timoteo mbaleyo,
2 kwa oyera mtima ndi abale okhulupirika mwa Kristu a m'Kolose: Cisomo kwa inu ndi mtendere wocokera kwa Mulungu Atate wathu.
3 Tiyamika Mulungu Atate wa Ambuye wathu Yesu Kristu ndi kupempherera Inu nthawi zonse,
4 popeza tidamva za cikhulupiriro canu ca mwa Kristu Yesu, ndi cikondi muli naco kwa oyera mtima onse;
5 cifukwa ca ciyembekezo cosungikira kwa inu m'Mwamba, cimene mudacimva kale m'mau a coonadi ca Uthenga Wabwino,
6 umene udafikira kwa inu; monganso m'dziko lonse lapansi umabala zipatso, numakula, monganso mwa inu; kuyambira tsikulo mudamva nimunazindildra cisomo ca Mulungu m'coonadi;
7 monga momwe munaphunzira kwa Epafra kapolo mnzathu wokondedwa, ndiyemtumiki wokhulupirika wa Kristu cifukwa ca ife;
8 amenenso anatifotokozera cikondi canu mwa Mzimu.
9 Mwa ici ifenso, kuyambira tsiku limene tidamva, sitileka kupembedzera ndi kupempherera inu, kuti mukadzazidwe ndi cizindikiritso ca cifuniro cace mu nzeru zonse ndi cidziwitso ca mzimu,
10 kuti mukayende koyenera Ambuye kukamkondweretsa monsemo, ndi kubala zipatso mu nchito yonse yabwino, ndi kukula m'cizindikiritso ca Mulungu;
11 olimbikitsidwa m'cilimbiko conse, monga mwa mphamvu ya ulemerero wace, kucitira cipiriro conse ndi kuleza mtima konse pamodzi ndi cimwemwe,
12 ndi kuyamika Atate, amene anatiyeneretsa ife kulandirana nao colowa ca oyera mtima m'kuunika;
13 amene anatilanditsa ife ku ulamuliro wa mdima, natisunthitsa kutilowetsa m'ufumu wa Mwana wa cikondi cace;
14 amene tiri nao maomboledwe mwa iye, m'kukhululukidwa kwa zocimwa zathu;
15 amene ali fanizo la Mulungu wosaonekayo, wobadwa woyamba wa cilengedwe conse;
16 pakuti mwa iye, zinalengedwa zonse za m'mwamba, ndi za padziko, zooneka ndi zosaonekazo, kapena mipando yacifumu, kapena maufumu, kapena maukulu, kapena maulamuliro; zinthu zonse zinalengedwa mwa iye ndi kwa iye.
17 Ndipo iye ali woyamba wa zonse, ndipo zonse zigwirizana pamodzi mwa iye.
18 Ndipo iye ali mutu wa thupi, Eklesiayo; ndiye ciyambi, wobadwa woyamba woturuka mwa akufa; kuti akakhale iye mwa zonse woyambayamba.
19 Pakuti kunamkomera Atate kuti mwa iye cidzalo conse cikhalire,
20 mwa Iyenso kuyanjanitsa zinthu zonse kwa iye mwini, atacita mtendere mwa mwazi wa mtanda wace; mwa Iyetu, kapena za padziko, kapena za m'mwamba.
21 Ndipo inu, okhala alendo kale ndi adani m'cifuwa canu m'nchito zoipazo, koma tsopano anakuyanjanitsani
22 m'thupi lace mwa imfayo, kukaimika inu oyera, ndi opanda cirema ndi osatsutsika pamaso pace;
23 ngatitu mukhalabe m'cikhulupiriro, ocirimika ndi okhazikika ndi osasunthika kulekana naco ciyembekezo ca Uthenga Wabwino umene mudaumva, wolalikidwa colengedwa conse ca pansi pa thambo; umene ine Paulo ndakhala mtumiki wace.
24 Tsopano 1 ndikondwera nazo zowawazo cifukwa ca inu, ndipo 2 ndikwaniritsa zoperewera za cisautso ca Kristu m'thupi langa 3 cifukwa ca thupi lace, ndilo Eklesiayo;
25 amene ndinakhala mtumiki wace, 4 monga mwa udindo wa Mulungu umene anandipatsa ine wakucitira inti, wakukwaniritsa mau a Mulungu,
26 5 ndiwo cinsinsico cinabisika kuyambira pa nthawizo, ndi kuyambira pa mibadwoyo; koma anacionetsa tsopano kwa oyera mtima ace,
27 kwa iwo amene Mulungu anafuna kuwazindikiritsa ici 6 cimene ciri cuma ca ulemerero wa cinsinsi pakati pa amitundu, ndiye Kristu mwa inu, ciyembekezo ca ulemerero;
28 amene timlalikira ife, ndi kucenjeza munthu ali yense 7 ndi kuphunzitsa munthu ali yense mu nzeru zonse, 8 kuti tionetsere munthu ali yense wamphumphu mwa Kristu;
29 kucita ici ndidzibvutitsa ndi kuyesetsa 9 monga mwa macitidwe ace akucita mwa ine ndi mphamvu.
1 Pakuti ndifuna kuti inu mudziwe nkhawa imene ndiri nayo cifukwa ca inu, ndi iwowa a m'Laodikaya, ndi onse amene sanaone nkhope yanga m'thupi;
2 kuti itonthozeke mitima yao, nalumikizike pamodzi iwo m'cikondi, kufikira cuma conse ca cidzalo ca cidziwitso, kuti akazindikire Iwo cinsinsi ca Mulungu, ndiye Kristu,
3 amene zolemera zonseza nzeru ndi cidziwitso zibisika mwa iye.
4 Ici ndinena, kuti munthu asakusokeretseni inu ndi mau okopakopa.
5 Pakuti ndingakhale ndiri kwina m'thupi, komatu mumzimu ndiri pamodzi ndi inu, wokondwera pakupenya makonzedwe anu, ndi cilimbiko ca cikhulupiriro canu ca kwa Kristu.
6 Cifukwa cace monga momwe munalandira Kristu Yesu Ambuye, muyende mwa iye,
7 ozika mizu ndi omangirika mwa iye, ndi okhazikika m'cikhulupiriro, monga munaphunzitsidwa, ndi kucurukitsa ciiyamiko.
8 Penyani kuti pasakhale wina wakulanda inu ngati cuma, mwa kukonda nzeru kwace, ndi cinyengo copanda pace, potsata mwambo wa anthu, potsata zoyamba za dziko lapansi, osati potsata Kristu;
9 pakuti mwa iye cikhalira cidzalo ca Umulungu m'thupi,
10 ndipo muli odzazidwa mwa iye, ndiye mutu wa ukulu wonse ndi ulamuliro;
11 amenenso munadulidwa mwa iye ndi mdulidwe wosacitika ndi manja, m'mabvulidwe a thupi, mu mdulidwe wa Kristu;
12 popeza munaikidwa m'manda pamodzi ndi iye muubatizo, momwemonso munaukitsidwa pamodzindi iye m'cikhulupiriro ca macitidwe a Mulungu, amene anamuukitsa iye kwa akufa.
13 Ndipo inu, pokhala akufa m'zolakwa ndi kusadulidwa kwa thupi lanu, anakupatsani moyo pamodzi ndi iye, m'mene adatikhululukira ife zolakwa zonse;
14 adatha kutifafanizira ca pa ifeco colembedwa m'zoikikazo, cimene cinali cotsutsana nafe; ndipo anacicotsera pakatipo, ndi kucikhomera ici pamtanda;
15 atabvula maukulu ndi maulamuliro, anawaonetsera poyera, nawagonjetsera nako.
16 Cifukwa cace munthu aliyense asakuweruzeni inu m'cakudya, kapena cakumwa, kapena m'kunena tsiku la phwando, kapena tsiku lokhala mwezi, kapena la Sabata;
17 ndizo mthunzi wa zirinkudzazo; koma thupi ndi la Kristu.
18 Munthu ali yense asakunyengeni ndi kulanda mphotho yanu ndi kudzicepetsa mwini wace, ndikugwadira kwa angelo, ndi kukhalira mu izi adaziona, wodzitukumula cabe ndi zolingalira za thupi lace, wosagwiritsa mutuwo,
19 kucokera kwa iye amene thupi lonse, lothandizidwa ndi kulumikizidwa pamodzi mwa mfundo ndi mitsempa, likula ndi makulidwe a Mulungu.
20 Ngati munafa pamodzi ndi Kristu kusiyana nazo zoyambaza dziko lapansi, mugonieranii ku zoikikazo, monga ngati moyo wanu mukhala nao m'dziko lapansi,
21 usaikapo dzanja, usalawa, usakhudza,
22 (ndizo zonse zakuonongedwa pocita nazo), monga mwa malangizo ndi maphunziro a anthu?
23 zimene ziri naotu manenedwe a nzeru m'kutumikira kwa cifuniro ca mwini wace, ndi kudzicepetsa, ndi kusalabadira thupi; koma ziribe mphamvu konse yakuletsa cikhutitso ca thupi.
1 Cifukwa cace ngati munaukitsidwa pamodzi ndi Kristu, funani zakumwamba, kumene kuli Kristu wokhala pa dzanja lamanja la Mulungu.
2 Lingalirani zakumwamba osati za padziko ai.
3 Pakuti munafa, ndipo moyo wanu wabisika pamodzi ndi Kristu mwa Mulungu,
4 Pamene Kristu adzaoneka, ndiye moyo wathu, pamenepo inunso mudzaonekera pamodzi ndi iye m'ulemerero.
5 Cifukwa cace fetsani ziwalozo ziri padziko; dama, cidetso, cifunitso ca manyazi, cilakolako coipa, nelicisiriro, cimene ciri kupembedza mafano;
6 cifukwa ca izi zomwe ukudza mkwiyo wa Mulungu pa ana a kusamvera;
7 zimene munayendamo inunso kale, pamene munakhala ndi moyo wanu m'menemo,
8 Koma tsopano tayani inunso zonsezi: mkwiyo, kupsa mtima, dumbo, mwano, zonyansa zoturuka m'kamwa mwanu:
9 musamanamizana wina ndi mnzace; popeza mudabvula munthu wakale pamodzi ndi nchito zace,
10 ndipo munabvala watsopano, amene alikukonzekawatsopano, kuti akhale naco cizindikiritso, mousa mwa cifaniziro ca iye amene anamlenga iye;
11 pamene palibe Mhelene ndi Ayuda, mdulidwe ndi kusadulidwa, wachedwa wakunja, Mskuti, kapolo, mfulu, komatu Kristu ndiye zonse, ndi m'zonse.
12 Cifukwa cace bvalani, monga osankhika a Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa, mtima wacifundo, kukoma mtima, kudzicepetsa, cifatso, kuleza mtima;
13 kulolerana wina ndi mnzace, ndi kukhululukirana eni okha, ngati wina ali naco cifukwa pa mnzace; monganso Ambuye anakhululukira inu, teroni inunso;
14 koma koposa izi zonse khalani naco cikondano, ndico comangira ca mtima wamphumphu.
15 Ndipo mtendere wa Kristu ucite ufumu m'mitima yanu, kulingakonso munaitanidwa m'thupi limodzi; ndipo khalani akuyamika.
16 Mau a Knstu akhalitse mwa inu cicurukire mu nzeru yonse, ndi kuphunzitsa ndi kuyambirirana eni okha ndi masalmo, ndimayamiko ndi nyimbo zauzimu, ndi kuyimbira Mulungu ndi cisomo mumtima mwanu.
17 Ndipo ciri conse mukacicita m'mau kapena muncbito, citani zonse m'dzina la Ambuye Yesu, ndi kuyamika Mulungu Atate mwa iye.
18 Akazi inu, muzimvera amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.
19 Amuna inu, kondani akazi anu, ndipo musawawire mtima iwo.
20 Ana inu, mverani akubala inu m'zonse, pakuti ici Ambuye akondwera naco.
21 Atate inu, musaputa ana anu, kuti angataye mtima.
22 Akapolo inu, mverani m'zonse iwo amene ali ambuye monga mwa thupi, wosati ukapolo wa pamaso, monga okondweretsa anthu, komatu ndi mtima wakulinga kumodzi, akuopa Ambuye;
23 ciri conse mukacicita, gwirani nchito mocokera mumtima, monga kwa Ambuye, osati kwa anthu ai;
24 podziwa kuti mudzalandira kwa Ambuye mphotho ya colowa; mutumikira Ambuye Kristu mwaukapolo.
25 Pakuti iye wakucita cosalungama adzalandiranso cosalungama anaeitaco; ndipo 1 palibe tsankhu.
1 Ambuye inu, citirani akapolo anu colungama ndi colingana; podziwa kuti inunso muli naye Mbuye m'Mwamba.
2 Citani khama m'kupemphera, nimudikire momwemo ndi ciyamiko;
3 ndi kutipempherera ifenso pomwepo, kuti Mulungu atitsegulire ife pakhomo pa mau, kuti tilankhule cinsinsi ca Kristu; cimenenso ndikhalira m'ndende,
4 kuti ndicionetse ici monga ndiyenera kulankhula.
5 Muyendere munzeru ndi iwo akunja, kucita macawi nthawi ingatayike.
6 Mau anu akhale m'cisomo, okoleretsa, kuti mukadziwe inu mayankhidwe anu a kwa yense akarani.
7 Zonse za kwa ine adzakuzindikiritsani Tukiko, mbale wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika ndi kapolo mnzanga mwa Ambuye:
8 amene ndamtuma kwa inu cifukwa ca ici comwe, kuti mukazindikire za kwa ife, ndi kuti atonthoze mitima yanu;
9 pamodzi ndi Onesimo, mbale wokhulupirika ndi wokondedwa, amene ali wa kwa inu. Zonse za kuno adzakuzindikiritsani inu.
10 Aristarko wam'ndende mnzanga akulankhulani inu ndi Marko, msuwani wa Bamaba (amene munalandira zolamulira za kwa iye; akafika kwanu, mumlandire iye),
11 ndi Yesu, wochedwa Yusto, ndiwo a mdulidwe; iwo okha ndiwo anchito anzanga a mu Ufumu wa Mulungu, ndiwo akundikhalira ine conditonthoza mtima.
12 Akulankhulani inu Epafra ndiye wa kwa inu ndiye kapolo wa Yesu Kristu, wakulimbira cifukwa ca inu m'mapemphero ace znasiku onse, kuti mukaime amphumphu ndi odzazidwa m'cifuniro conse ca Mulungu.
13 Pakuti ndimcitira iye umboni kuti adziwawitsa nayo nchito cifukwa ca inu, ndi iwo a m'Laodikaya, ndi iwo a m'Herapoli.
14 Akulankhulani inu Luka sing'anga wokondedwa, ndi Dema.
15 Lankhulani abalewo a m'Laodikaya, ndi Numfa, ndi Mpingowo wa m'nyumba yao.
16 Ndipo pamene mudamwerenga kalata uyu, amwerengenso mu Mpingo wa ku Laodikaya, ndi inunso muwerenge wa ku Laodikaya,
17 Ndipo nenani kwa Arkipo, Samaliratu utumiki umene udaulandira mwa Ambuye, kuti uukwanitse.
18 Kulankhula ndi dzanja langa, kwa ine Paulo. Kumbukilani zoo mangira zanga, Cisomo cikhale nanu.