1

1 NDIPO atafa Mose mtumiki wa Yehova, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mnyamata wa Mose,

2 Mose mtumiki wanga wafa; tauka tsono, nuoloke Yordano uyu, iwe ndi anthu awa onse, kulowa m'dzikomo ndirikuwapatsa, ndiwo ana a Israyeli.

3 Pali ponse phazi lanu lidzapondapo ndinakupatsani, monga ndinanena ndi Mose.

4 Kuyambira cipululu, ndi Lebano uyu, kufikira mtsinje waukulu mtsinje wa Firate, dziko lonse la Ahiti, ndi kufikira nyanja yaikuru ku malowero a dzuwa, ndiwo malire anu.

5 Palibe munthu adzatha kuima pamaso pako masiku onse a moyo wako; monga ndinakhala ndi Mose momwemo ndidzakhala ndi iwe; sindidzakusowa, sindidzakusiya.

6 Khala wamphamvu, nulimbike mtima, pakuti udzagawira anthu awa dzikoli likhale colowa cao, ndilo limene ndinalumbirira makolo ao kuwapatsa.

7 Komatu khala wamphamvu, nulimbike mtima kwambiri, kuti usamalire kucita monga mwa cilamulo conse anakulamuliraco Mose mtumiki wanga; usacipambukire ku dzanja lamanja kapena kulamanzere, kuti ukacite mwanzeru kuli konse umukako.

8 Buku ili la cilamulo lisacoke pakamwa pako; koma ulingiriremo usana ndi usiku, kuti usamalire kucita monga mwa zonse zolembedwamo; popeza ukatero udzakometsa njira yako, nudzacita mwanzeru.

9 Kodi sindinakulamulira iwe? Khala wamphamvu, nulimbike mtima, usaope, kapena kutenga nkhawa, pakuti Yehova Mulungu wako ali ndi iwe kuli konse umukako.

10 Pamenepo Yoswa analamulira akapitao a anthu, ndi kuti,

11 Pitani pakati pa cigono, nimulamulire anthu, ndi kuti, Mudzikonzeretu kamba, pakuti asanapite masiku atatu mudzaoloka Yordano uyu, kulowa ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, likhale lanu lanu.

12 Ndipo Yoswa anati kwa Arubeni, ndi Agadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati, ndi kuti,

13 Kumbukilani mau amene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulirani inu, kuti, Yehova Mulungu wanu akupatsani mpumulo, nadzakupatsani dziko lino.

14 Akazi anu, ana anu, ndi zoweta zanu zikhale m'dzikoli anakuninkhani Mose, tsidya lino la Yordano; koma inu muoloke okonzeka kunkhondo pamaso pa abale anu, ngwazi zonse, ndi kuwathandiza;

15 mpaka Yehova atapatsa abale anu mpumulo, monga umo anakuninkhirani inu, naonso alandira dzikolo awaninkha Yehova Mulungu wanu; pamenepo mubwerere ku dziko lanu lanu, ndi kukhala nalo, limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya lino la Yordano la kum'mawa,

16 Ndipo anamyankha Yoswa, nati, Zonse mwatilamulira tidzacita, ndipo kuli konse mutitumako tidzamuka.

17 Monga momwe tinamvera mau onse a Mose momwemo tidzamvera inu; komatu akhale ndi inu Yehova Mulungu wanu monga anakhala ndi Mose.

18 Ali yense wakupikisana ndi inu, osamvera mau anu muli monse mukamlamulira, aphedwe; komatu khalani wamphamvu, nimulimbike mtima.

2

1 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, ali ku Sitimu, anatuma amuna awiri mosadziwika kukazonda, ndi kuti, Mukani, mulipenye dzikolo, ndi ku Yeriko. Ndipo anamuka nalowa m'nyumba ya mkazi wadama, dzina lace Rahabi, nagona momwemo.

2 Ndipo wina anaiuza mfumu ya Yeriko, kuti, Taonani, usiku uno alowa muno amuna a ana a Israyeli, kulizonda dziko.

3 Ndipo mfumu ya Yeriko inatuma wina kwa Rahabi, ndi kuti, Turutsa amunawo anafika kwanu, amene analowa m'nyumba mwako; popeza anadzera kulizonda dziko lonse.

4 Koma mkaziyo anatenga amuna awiriwo, nawabisa; natero, Inde, amunawo anandifikira; koma sindinadziwa uko afuma;

5 ndipo m'mene akadati atseke pacipata, kutada, anaturuka amunawo; uko anamuka amunawo osakudziwa ine; muwalondole msanga, pakuti mudzawapeza.

6 Koma adawakweretsa patsindwi, nawabisa ndi mitengo yanthamza yoyanika patsindwi.

7 Ndipo amunawo anawalondola pa njira ya ku Yordano yomka kudooko; ndipo ataturuka akuwalondola, anatseka pacipata.

8 Koma asanagone iwo, anawakwerera patsindwi iye,

9 nati kwa amunawo, Ndidziwa kuti Yehova wakupatsani dzikoli, ndi kuti kuopsa kwanu kwatigwera, ndi kuti okhala m'dziko onse asungunuka pamaso panu.

10 Popeza tidamva kuti Yehova anaphwetsa madzi a m'Nyanja Yofiira pamaso panu, muja mudaruruka m'Aigupto; ndi cija munacitira mafumu awiri a Aamori okhala tsidya la Yordano, ndiwo Sihoni ndi Ogi, amene mudawaononga konse.

11 Ndipo titamva ici mitima yathu inasungunuka; anahbenso mtima ndi mmodzi yense, cifukwa ca inu; pakuti Yehova Mulungu wanu, ndiye Mulungu wa m'mwamba umo, ndi pa dziko lapansi.

12 Ndipo tsopano, mundilumbiriretu kwa Yehova, popeza ndakucitirani cifundo, kuti inunso mudzacitira cifundo a m'nyumba ya atate wanga ndi kundipatsa cizindikilo coona,

13 kuti mudzawasunga ndi moyo atate wanga ndi mai wanga, ndi alongo anga ndi abale anga, ndi zonse ali nazo, ndi kupulumutsa miyoyo yathu kuimfa.

14 Ndipo amunawo anati kwa iye, Moyo wathu ndiwo moyo wanu, mukapanda kuulula codzera ife; ndipo kudzakhala kuti, pakutipatsa ife dziko ili Yehova, tidzakucitira cifundo ndi coonadi.

15 Pamenepo anawatsitsa pazenera ndi cingwe; popeza nyumba yace lnali pa linga La mudzi, nakhala iye palingapo.

16 Ndipo anati kwa iwo, Mukani kuphiri, olondola angakupezeni; mubisale kumeneko masiku atatu, mpaka atabwerera olondolawo, pamenepo muyende ulendo wanu.

17 Ndipo amunawo anati kwa iye, Sitidzacimwira lumbiro lako ili watilumbiritsali.

18 Taona, tikadzalowa m'dzikomo ife, uzimanga cingwe ici cofiira pazenera pamene watitsitsira; ndipo udzasonkhanitsa m'nyumbamo atate wako ndi mai wako nui abale ako ndi a m'nyumba onse a atate wako.

19 Ndipo kudzakhala kuti ali yense akadzaturuka pa khomo la nyumba yako kubwalo, imfa imeneyi ndi yace, tiribe kuparamula ife; koma ali yense adzakhala ndi iwe m'nyumba, likamfikira dzanja, imfa imeneyi ndi yathu.

20 Koma ukaulula codzera ifeco tidzamasukira lumbiro lako watilumbiritsali.

21 Nati iye, Momwemo, monga mwa mau anu. Ndipo anawauza amuke, iwo namuka; namanga iye cingwe cofiiraco pazenera.

22 Ndipo anayenda iwo, nafika kuphiri, nakhalako masiku atatu mpaka atabwerera olondolawo; popeza olondolawo anawafunafuna panjira ponse, osawapeza.

23 Pamenepo amuna awiriwo anabwerera, natsika m'phirimo naoloka, nafika kwa Yoswa mwana wa Nuni, namfotokozera zonse zidawagwera.

24 Ndipo anati kwa Yoswa, Zoonadi, Yehova wapereka dziko lonse m'manja mwathu; ndiponso nzika zonse zasungunuka pamaso pathu.

3

1 Ndipo Yoswa analawirira mamawa, kucoka ku Sitimu, nafika ku Yordano, iye ndi ana onse a Israyeli; nagona komweko, asanaoloke.

2 Ndipo kunali atapita masiku atatu, akapitao anapita pakati pa cigono;

3 nalamulira anthu, ndi kuti, Mukadzaona likasa la cipangano la Yehova Mulungu wanu, ndi ansembe Aleviwo atalisenza, pamenepo mucoke kwanu ndi kulitsata.

4 Koma pakhale dera pakati pa inu ndi ilo, monga mikono zikwi ziwiri poliyesa; musaliyandikire, kuti mudziwe njira imene muziyendamo; popeza simunapita njirayi kufikira lero.

5 Ndipo Yoswa ananena kwa anthu, Mudzipatule, pakuti mawa Yehova adzacita zodabwiza pakati pa inu.

6 Ndipo Yoswa anati kwa ansembe, Senzani likasa la cipangano, nimuoloke pamaso pa anthu. Nasenza iwo likasa la cipangano, natsogolera anthu.

7 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, Lero lino ndidzayamba kukukuza pamaso pa Aisrayeli onse, kuti adziwe, kuti monga momwe ndinakhalira ndi Mose, momwemo ndidzakhala ndi iwe.

8 Ndipo uzilamulira ansembe akunyamula likasa la cipangano, ndi kuti, Pamene mufika kumphepete kwa madzi a Yordano muziima m'Yordano.

9 Ndipo Yoswa anati kwa ana a Israyeli, Idzani kuno, mumve mau a Yehova Molungu wanu.

10 Nati Yoswa, Ndi ici mudzadziwa kuti Mulungu wamoyo ali pakati pa inu, ndi kuti adzapitikitsa ndithu pamaso panu Akanani, ndi Ahiti, ndi Ahivi, ndi Aperizi, ndi Agirigasi, ndi Aamori, ndi Ayebusi.

11 Taonani, likasa la cipangano La Ambuye wa dziko lonse lapansi lioloka Yordano pamaso panu,

12 Ndipo tsono, mudzitengere amuna khumi ndi awiri mwa mapfuko a Israyeli, pfuko limodzi mwamuna mmodzi.

13 Ndipo kudzakhala, akaima mapazi a ansembe akusenza likasa la Yehova Ambuye wa dziko lonse, m'madzi a Yordano, adzadulidwa madziwo, ndiwo madzi ocokera kumagwero, nadzaima mulu umodzi.

14 Ndipo kunali pocoka anthu ku mahema ao kukaoloka Yordano, ansembe anasenza likasa la cipangano pamaso pa anthu.

15 Ndipo pamene iwo akusenza likasa anafika ku Yordano, nathibika m'mphepete mwa madzi mapazi a ansembe akusenza likasa, pakuti Yordano asefuka m'magombe ace onse, nyengo yonse ya masika,

16 pamenepo madzi ocokera kumagwero anaima, nauka ngati mulu, kutalitu ku Adamu, ndiwo mudzi wa ku mbali ya Zaretani; koma madzi akutsikira kumka ku nyanja ya cidikha, ndiyo Nyanja ya Mcere, anadulidwa konse; ndipo anthu anaoloka pandunji pa Yeriko.

17 Ndipo ansembe akulisenza likasa la cipangano la Yehova, anaima pouma pakati pa Yordano, ndi Aisrayeli onse anaoloka pouma mpaka mtundu wonse unatha kuoloka Yordano.

4

1 Ndipo kunali, utatha kuoloka Yordano mtundu wonse, Yehova ananena ndi Yoswa, nati,

2 Mudzitengere mwa anthu, amuna khumi ndi awiri, pfuko limodzi mwamuna mmodzi;

3 ndipo muwalamulire iwo ndi kuti, Mudzitengere pano pakati pa Yordano, poimapo mapazi a ansembe, miyala khumi ndi iwiri, ndi kuoloka nayo, ndi kulika m'mogona m'mene mugonamo usiku uno.

4 Pamenepo Yoswa anaitana amuna khumi ndi awiriwo amene anawaikiratu mwa ana a Israyeli, pfuko limodzi mwamuna mmodzi;

5 nanena nao Yoswa, Olokani, kutsogolera likasa la Yehova Mulungu wanu pakati pa Yordano, nimudzisenzere yense mwala paphewa pace, monga mwa kuwerenga kwa mapfuko a ana a Israyeli;

6 kuti ici cikhale cizindikilo pakati pa inu. Akakufunsani ana anu m'tsogolomo, ndi kuti, Miyala iyi nja ciani ndi inu?

7 munene nao, Cifukwa madzi a Yordano anadulidwa patsogolo pa likasa la cipangano ca Yehova; muja lidaoloka Yordano, madzi a Yordano anadulidwa; ndipo miyala iyi idzakhala cikumbutso ca ana a Israyeli cikhalire.

8 Ndipo ana a Israyeli anacita monga Yoswa anawalamulira, nasenza miyala khumi ndi iwiri pakati pa Yordano, monga Yehova adalankhula ndi Yoswa, monga mwa kuwerenga kwa mapfuko a ana a Israyeli; ndipo anaoloka nayo kumka kogona, naiika komweko.

9 Ndipo Yoswa anaimika miyala khumi ndi iwiri pakati pa Yordano, poimapo mapazi a ansembe akusenza likasa la cipangano; ikhala komweko kufikira lero lino.

10 Pakuti ansembe akusenza likasa anaima pakati pa Yordano, mpaka zitatha zonse Yehova adazilamulira Yoswa anene kwa anthu, monga mwa zonse Mose adalamulira Yoswa; ndipo anthu anafulumira kuoloka.

11 Ndipo kunali, atatha kuoloka anthu onse, likasa la Yehova linaoloka, ndi ansembe, pamaso pa anthu.

12 Ndipo ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi gawo lija la pfuko la Manase anaoloka ndi zida zao pamaso pa ana a Israyeli, monga Mose adanena nao;

13 ngati zikwi makumi anai ankhondo okonzeka anaoloka pamaso pa Yehova kuthira nkhondo ku zidikha za Yeriko.

14 Tsiku lomwelo Yehova anakulitsa Yoswa pamaso pa Aisrayeli onse; ndipo anamuopa monga anaopa Mose, masiku onse amoyowace.

15 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa,

16 Lamulira ansembe akusenza likasa la umboni, kuti akwere kuturuka m'Yordano.

17 Pamenepo Yoswa analamulira ansembe, ndi kuti, Kwerani kuturuka m'Yordano.

18 Ndipo kunali, atakwera ansembe akusenza likasa la cipangano la Yehova, kuturuka pakati pa Yordano, nakwera pamtunda mapazi a ansembe, madzi a m'Yordano anabwera m'njira mwace, nasefuka m'magombe ace onse monga kale.

19 Ndipo anthu anakwera kuturuka m'Yordano tsiku lakhumi la mwezi woyamba, namanga misasa ku Giligala, mbali ya ku m'mawa kwa Yeriko.

20 Ndipo Yoswa anaimika ku Giligala miyala ija khumi ndi iwiri adaitenga m'Yordano.

21 Ndipo anati kwa ana a Israyeli, Ana anu akadzafunsa atate ao masiku akudza, ndi kuti, Miyala iyi nja ciani?

22 pamenepo muzidziwitsa ana anu, ndi kuti, Israyeli anaoloka Yordano uyu pouma.

23 Pakuti Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yordano pamaso panu, mpaka mutaoloka; monga Yehova Mulungu wanu anacitira Nyanja Yofiira, imene anaiphwetsa pamaso pathu, mpaka titaoloka;

24 kuti mitundu yonse ya pa dziko lapansi idziwe dzanja la Yehova, kuti ndilo lamphamvu; kuti lope Yehova Mulungu wanu masiku onse.

5

1 Ndipo kunali, pamene mafumu onse a Aamori okhala tsidya la kumadzulo la Yordano, ndi mafumu onse a Akanani okhala ku Nyanja ya Mcere anamvakuti Yehova anaphwetsa madzi a Yordano pamaso pa ana a Israyeli mpaka titaoloka, mtima wao unasungunuka, analibenso moyo cifukwa ca ana a Israyeli.

2 Nthawi imeneyo Yehova anati kwa Yoswa, Udzisemere mipeni yamiyala, nudulenso ana a Israyeli kaciwiri.

3 Ndipo Yoswa anadzisemera mipeni yamiyala nadula ana a Israyeli pa Gibeya Naraloti.

4 Koma cifukwa cakuti Yoswa anawadula ndi ici: anthu onse oturuka m'Aigupto, anthu amuna, ndiwo amuna onse ankhondo, adafa m'cipululu panjira, ataturuka m'Aigupto.

5 Pakuti anthu onse anaturukawo anadulidwa; koma anthu onse obadwa m'cipululu panjira poturuka m'Aigupto sanadulidwa.

6 Pakuti ana a Israyeli anayenda m'cipululu zaka makumi anai, mpaka mtundu wonse wa amuna ankhondo oturuka m'Aigupto udatha, cifukwa ca kusamvera mau a Yehova; ndiwo amene Yehova anawalumbirira kuti sadzawaonetsa dziko limene Yehova analumbirira makolo ao kudzatipatsa, ndilo dziko moyenda mkaka ndi uci.

7 Koma ana ao amuna amene anawautsa m'malo mwao, iwowa Yoswa anawadula; popeza anakhala osadulidwa, pakuti sanawadula panjira.

8 Ndipo kunali, atatha kudula mtundu wonse, anakhala m'malo mwao m'cigono mpaka adacira.

9 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, Lero Uno ndakukunkhunizirani mtonzo wa Aigupto, Cifukwa cace dzina la malowo analicha Giligala kufikira lero lino.

10 Ndipo ana a Israyeli anamanga misasa ku Giligala; nacita Paskha tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi, madzulo, m'zidikha za Yeriko.

11 Ndipo m'mawa mwace atatha Paskha, anadya tirigu wakhwimbi wa m'dziko, mikate yopanda cotupitsa ndi tirigu wokazinga tsiku lomwe lija.

12 Koma m'mawa mwace mana analeka, atadya iwo tirigu wakhwimbi wa m'dziko; ndipo ana a Israyeli analibenso mana; koma anadya zipatso za dziko la Kanani caka comwe cija.

13 Ndipo kunali, pokhala Yoswa ku Yeriko, anakweza maso ace, napenya, ndipo taona, panaima muthu pandunji pace ndi lupanga lace losolola m'dzanja lace; namuka Yoswa kuli iye, nati iye, Ubvomerezana ndi ife kapena ndi aelani athu?

14 Nati, lai, koma ndadza ine, kazembe wa ankhondo a Yehova. Pamenepo Yoswa anagwa nkhope yace pansi, napembedza, nati kwa iye, Anenanji Ambuyanga kwa mtumiki wace?

15 Ndipo kazembe wa ankhondo a Yehova anati kwa Yoswa, Bvula nsapato yako pa phazi lako; pakuti malo upondapo mpopatulika. Nacita Yoswa comweco.

6

1 Koma ku Yeriko anatseka pazipata, natsekedwa cifukwa ca ana a Israyeli, panalibe woturuka, panalibenso wolowa.

2 Ndipo Yehova ananena kwa Yoswa, Taona, ndapereka m'dzanja lako Yeriko ndi mfumu yace, ndi ngwazi zace.

3 Ndipo muzizungulira mudzi Inu nonse ankhondo, kuuzungulira mudzi kamodzi. Muzitero masiku asanu ndi limodzi.

4 Ndipo ansembe asanu ndi awiri azinyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga: za nkhosa zamphongo, natsogolere nazo likasa; koma tsiku lacisanu ndi ciwiri muzizungulira mudziwo kasanu ndi kawirio ndi ansembe aziliza mphalasazo.

5 Ndipo kudzakhala kuti akaliza cilizire ndi nyanga ya nkhosa yamphongo, nimumva kulira kwa mphalasa, anthu onse apfuule mpfuu yaikuru; ndipo linga la mudziwo lidzagwa pomwepo, ndi anthu adzakwera ndi kulowamo yense kumaso kwace.

6 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anaitana ansembe, nanena nao, Senzani likasa la cipangano, ndi ansembe asanu ndi awiri anyamule mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo, kutsogolera nazo likasa la Yehova.

7 Nati kwa anthu, Pitani, muzizungulira mudzi, ndi ankhondo ndi zida zao atsogolere likasa la Yehova.

8 Ndipo atanena kwa anthu Yoswa, ansembe asanu ndi awiri akunyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo pamaso pa Yehova, anapita naliza mphalasazo; ndipo likasa la cipangano ca Yehova linawatsata.

9 Ndipo okonzeka kunkhondo anatsogolera ansembe akuliza mphalasa, koma akudza m'mbuyo anatsata likasa, ansembe ali ciombere poyenda iwo.

10 Ndipo Yoswa analamulira anthu, ndi kuti, Musamapfuula, kapena kumveketsa mau anu, asaturuke konse mau m'kamwa mwanu, mpaka tsiku lakunena nanu ine, Pfuulani; pamenepo muzipfuula.

11 Ndipo anazungulitsa likasa la Yehova mudzi, kuzungulira kamodzi; pamenepo analowa kucigono, nagona m'mwemo.

12 Ndipo Yoswa analawira mamawa, ndi ansembe anasenza likasa la Yehova.

13 Ndipo ansembe asanu ndi awiri, akunyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo ndi kutsogolera nazo likasa la Yehova, anayenda ciyendere naliza mphalasazo; ndi okonzeka kunkhondowo anawatsogolera, ndi akudza m'mbuyo anatsata likasa la Yehova, ansembe ali ciombere poyenda iwo.

14 Ndipo tsiku laciwiri anazungulira mudzi kamodzi, nabwera kucigono; anatero masiku asanu ndi limodzi.

15 Ndipo kunali, tsiku lacisanu ndi ciwiri analawira mamawa, mbandakuca, nazungulira mudzi mommuja kasanu ndi kawiri; koma tsiku lijalo anazungulira mudzi kasanu ndi kawiri.

16 Ndipo kunali, pa nthawi yacisanu ndi ciwiri, pamene ansembe analiza mphalasa, Yoswa anati kwa anthu, Pfuulani; pakuti Yehova wakupatsani mudziwo.

17 Koma mudziwo udzaperekedwa kwa Yehova ndi kuonongeka konse, uwu ndi zonse ziri m'mwemo; Rahabi yekha wadamayo adzakhala ndi moyo, iye ndi onse ali naye m'nyumba, cifukwa anabisa mithenga tinawatumawo.

18 Ndipo inu, musakhudze coperekedwaco, mungadziononge konse, potapa coperekedwaco; ndi kuononga konse cigono ca Israyeli ndi kucisautsa.

19 Koma siliva yense, ndi golidi yense, ndi zotengera za mkuwa ndi citsulo zikhala copatulikira Yehova; zilowe m'mosungira cuma ca Yehova.

20 Ndipo anthu anapfuula, naliza mphalasa ansembe; ndipo kunali, pamene anthu anamva kulira kwa mphalasa, anapfuula anthu ndi mpfuu yaikuru, niligwa linga pomwepo; nakwera anthu kulowa m'mudzi, yense kumaso kwace; nalanda mudziwo.

21 Ndipo anapereka kuziononga ndi lupanga lakuthwa zonse za m'mudzi, amuna ndi akazi omwe, ana ndi nkhalamba zomwe, kudza ng'ombe, ndi nkhosa, ndi aburu, ndi lupanga lakuthwa.

22 Ndipo Yoswa ananena kwa amuna awiri anazonda dzikowo, Lowani m'nyumba ya mkazi wadamayo, ndi kuturutsamo mkaziyo ndi zonse ali nazo, monga munamlumbirira iye.

23 Pamenepo anyamata ozondawo analowa, naturutsa Rahabi, ndi atate wace ndi mai wace ndi abale ace, ndi onse anali nao; anaturutsanso acibale ace onse; nawaika kunja kwa cigono ca Israyeli.

24 Ndipo anatentha mudzi ndi moto, ndi zonse zinali m'mwemo; koma siliva ndi golidi ndi zotengera zamkuwa ndi zacitsulo anaziika m'mosungira cuma ca nyumba ya Yehova.

25 Koma Rahabi, mkazi wadamayo ndi banja la atate wace, ndi onse anali nao, Yoswa anawasunga ndi moyo; ndipo anakhala pakati pa Israyeli mpaka lero tino; cifukwa anabisa mithenga imene Yoswa anaituma kuzonda Yeriko.

26 Ndipo Yoswa anawalumbirira nyengo ija, ndi kuti, Wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzauka ndi kumanga mudzi uwu wa Yeriko; adzamanga kuzika kwace ndi kutayapo mwana wace woyamba, nadzaimika zitseko zace ndi kutayapo mwana wace wotsirizira.

27 Potero Yehova anakhala ndi Yoswa; ndi mbiri yace inabuka m'dziko lonse.

7

1 Koma ana a Israyeli analakwa ndi coperekedwaco; popeza Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa pfuko la Yuda, anatapa coperekedwaco; ndi mkwiyo wa Yehova unayakira ana a Israyeli.

2 Ndipo Yoswa anatuma amuna kucokera ku Yeriko apite ku Ai, ndiwo pafupi pa Beti-aveni, kum'mawa kwa Beteli; nanena nao, Kwerani ndi kukazonda dziko. Nakwera amunawo, nazonda Ai.

3 Ndipo anabwera kwa Yoswa, nati kwa iye, Asakwere anthu onse; koma akwere amuna ngati zikwi ziwiri kapena zitatu kukantha Ai; musalemetsa anthu onse kumkako, pakuti a komweko ndi owerengeka;

4 Potero mwa anthu anakwerako amuna monga zikwi zitatu; koma anathawa pamaso pa amuna a ku Ai.

5 Ndipo amuna a ku Ai anawakantha amuna, ngati makumi atatu mphambu asanu ndi mmodzi; nawapitikitsa kuyambira pacipata mpaka ku Sebarimu, nawakantha potsika; ndi mitima ya anthu inasungunuka inga madzi.

6 Ndipo Yoswa anang'amba zobvala zace, nagwa nkhope yace pansi, ku likasa la Yehova, mpaka madzulo, iye ndi akulu akulu a Israyeli, nathira pfumbi pamitu pao.

7 Ndipo Yoswa anati, Ha! Ambuye, Yehova, mwaolotseranji anthu awa pa Yordano, kutipereka ife m'dzanja la Aamori, kutiononga ife? mwenzi titalola ndi kukhala tsidya lija la Yordano!

8 Ndidzanenanji, Ambuye, Israyeli atabwerera m'mbuyo pamaso pa adani ao?

9 Akadzamva ici Akanani ndi okhala m'dziko onse, adzatizinga ndi kuduliratu dzina lathu pa dziko lapansi; ndipo mudzacitiranji dzina lanu lalikuru?

10 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, Tauka, wagweranji pankhope pako cotere?

11 Israyeli wacimwa, nalakwiranso cipangano canga, ndinawalamuliraco; natengakonso coperekedwaco; anabanso, nanyenganso, naciika pakati pa akatundu ao.

12 Mwa ici ana a Israyeli sangathe kuima pamaso pa adani ao, awafulatira adani ao, pakuti aperekedwa aonongeke. Sindidzakhalanso nanu mukapanda kuononga coperekedwaco, kucicotsa pakati pa inu.

13 Tauka, patula anthu, nuti, Mudzipatulire mawa; pakuti atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Pali coperekedwa cionongeke pakati pako, Israyeli iwe; sukhoza kuima pamaso pa adani ako, mpaka mutacotsa coperekedwaco pakati panu.

14 Koma m'mawa adzakuyandikitsani, pfuko ndi pfuko; ndipo kudzali kuti pfukoli Yehova aliulula lidzayandikira mwa zibale zace; ndi cibale Yehova aciulula cidzayandikira monga mwa a nyumba ace; ndi a m'nyumbawo Yehova awaulula adzayandikira mmodzi mmodzi.

15 Ndipo kudzali kuti iye wogwidwa ali naco coperekedwaco adzatenthedwa ndi moto, iye ndi zonse ali nazo cifukwa analakwira cipangano ca Yehova, ndi cifukwa anacita copusa m'Israyeli.

16 Ndipo Yoswa analawira mamawa, nayandikizitsa Israyeli, pfuko ndi pfuko; ndi pfuko la Yuda linagwidwa;

17 nayandikizitsa zibale za Yuda, nagwira cibale ca Azari; nayandikizitsa cibale ca Azari, mmodzi mmodzi, nagwidwa Zabidi;

18 nayandikizitsa a m'nyumba yace mmodzi mmodzi; ndipo Akani, mwana wa Karimu, mwanu wa Zabidi, mwana wa Zera, wa pfuko la Yuda anagwidwa.

19 Ndipo Yoswa anati kwa Akani, Mwana wanga, ucitiretu ulemu Yehova Mulungu wa Israyeli, numlemekeze iye; nundiuze tsopano, wacitanji? usandibisire.

20 Ndipo Akani anayankha Yoswa nati, Zoonadi, ndacimwira Yehova Mulungu wa Israyeli, ndacita zakuti zakuti;

21 pamene ndinaona pazofunkha maraya abwino a ku Babulo, ndi masekeli mazana awiri a siliva, ndi cikute cagolidi, kulemera kwace masekeli makumi asanu, ndinazikhumbira ndi kuzitenga; ndipo taonani, ndazibisa m'nthaka pakati pa hema wanga, ndi siliva pansi pacepo.

22 Pamenepo Yoswa anatuma mithenga, iwo nathamangira kuhema; ndipo taonani, zidabisika m'hema mwace ndi siliva pansi pace.

23 Ndipo anazicotsa pakati pa hema, nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa ana onse a Israyeli, nazitula pamaso pa Yehova.

24 Ndipo Yoswa, ndi Aisrayeli onse naye, anatenga Akani mwana wa Zera, ndi siliva, ndi marayawo, ndi cikute cagolidi, ndi ana ace amuna ndi akazi, ndi ng'ombe zace, ndi aburu ace, ndi nkhosa zace, ndi hema wace ndi zace zonse; nakwera nazo ku cigwa ca Akori.

25 Ndipo Yoswa anati, Watisautsiranji? Yehova adzakusautsa lero lino. Ndipo, Aisrayeli onse anamponya miyala, nawatentha ndi moto, nawaponya miyala.

26 Ndipo anamuuniikira mulu waukuru wamiyala, wokhalako kufikira lero lino; ndipo Yehova anatembenuka kusiya mkwiyo wace waukuru. Cifukwa cace anacha dzina lace la malowo, Cigwa ca Akori, mpaka lero lino.

8

1 Pamenepo Yehova anati kwa Yoswa, Usaope, kapena kutenga nkhawa, tenga anthu onse a nkhondo apite nawe, ndipo tauka, kwera ku Ai; taona, ndapereka m'dzanja lako mfumu ya ku Ai, ndi anthu ace ndi mudzi wace ndi dziko lace;

2 ndipo uzimcitira Ai ndi mfumu yace monga umo unamcitira Yeriko ndi mfumu yace; koma zofunkha zace ndi ng'ombe zace mudzifunkhire nokha; udziikire anthu aja lire kukhonde kwa mudzi.

3 Pamenepo anauka Yoswa, ndi anthu onse a nkhondo, kuti akwere ku Ai; ndipo Yoswa anasankha amuna zikwi makumi atatu, ndiwo ngwazi, nawatumiza apite usiku,

4 nawalamulira ndi kuti, Taonani, muzikhala olalira kukhonde kwa mudzi; musakhalira kutali ndi mudzi, koma mukhale okonzekeratu nonse;

5 ndipo ine, ndi anthu onse ali nane, tidzayandikira mudzi; ndipo kudzali, pamene aturuka kudzakomana nafe, monga poyamba paja, tidzathawa pamaso pao;

6 ndipo adzaturuka kutitsata mpaka tidawakokera asiyane ndi mudzi; pakuti adzanena, Atithawa pamaso pathu monga poyamba pala; nafenso tidzathawa pamaso pao;

7 pamenepo muziuka m'molalira ndi kulowa m'mudzi; pakuti Yehova Mulungu wanu adzaupereka m'manja mwanu.

8 Ndipo kudzali, mutagwira mudzi, muzitentha mudziwo ndi moto; muzicita monga mwa mau a Yehova; taonani, ndakulamulirani.

9 Ndipo Yoswa anawatuma, namuka iwo kulowa m'molalira, nakhala pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai; koma Yoswa anakhala mwa anthu usiku uja.

10 Ndipo Yoswa analawira mamawa, nayesa anthu, nakwera, iye ndi akuru a Israyeli, pamaso pa anthu a ku Ai.

11 Ndi anthu onse a nkhondo okhala naye anakwera, nayandikira nafika pamaso pa mudzi, namanga misasa kumpoto kwa Ai; koma pakati pa iye ndi Ai panali cigwa.

12 Ndipo anatenga amuna ngati zikwi zisanu, nawaika m'molalira pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa mudzi.

13 Momwemo anaika anthu, khamu lonse lokhala kumpoto kwa mudzi, ndi olalira ao kumadzulo kwa mudzi, ndipo usiku uja Yoswa analowa pakati pa cigwa,

14 Ndipo kunali, pamene mfumu ya ku Ai anaciona, anafulumira iwo, nalawira mamawa, naturuka amuna a m'mudzi kuthirana ndi Israyeli, iye ndi anthu ace onse, poikidwiratu patsogolo pa cidikha; popeza sanadziwa kuti amlalira kukhonde kwa mudzi.

15 Ndipo Yoswa ndi Aisrayeli onse anaoneka ngati a ku Ai alikuwathyola, nathawira njira ya kucipululu.

16 Pamenepo anthu onse okhala m'mudzi, anaitanidwa awapitikitse, nampitikitsa Yoswa, nakokedwa kusiyana ndi mudzi.

17 Ndipo sanatsala mwamuna mmodzi yense m'Ai kapena m'Beteli osaturukira kwa Israyeli; nasiya mudzi wapululu, napitikitsa Israyeli.

18 Pamenepo Yehova anati kwa Yoswa, Tambasula nthungo iri m'dzanja lako iloze ku Ai, pakuti ndidzaupereka m'dzanja lako. Ndipo Yoswa anatambasula nthungoyo inali m'dzanja lace kuloza mudzi.

19 Nauka msanga olalirawo m'mbuto mwao, nathamanga pamene anatambasula dzanja lace, nalowa m'mudzi, naugwira; nafulumira nayatsa mudziwo.

20 Pamene amuna a ku Ai anaceuka, anapenya, ndipo taonani, utsi wa mudzi unakwera kumwamba; nasowa mphamvu iwo kuthawa cakuno kapena cauko; ndi anthu othawira kucipululu anatembenukira owapitikitsa.

21 Ndipo pakupenya Yoswa ndi Israyeli yense kuti olalirawo adagwira mudzi, ndi kuti utsi wa mudzi unakwera, anabwerera, nawapha amuna a ku Ai.

22 A kumudzinso anawaturukira; potero anakhala pakati pa Israyeli, ena mbali yina, ena mbali yina; ndipo anawakantha, mpaka sanatsala kapena kupulumuka wa iwo ndi mmodzi yense.

23 Koma mfumu ya ku Ai anamgwira wamoyo, nadza naye kwa Yoswa.

24 Ndipo kunali, atatha Israyeli kupha nzika zonse za ku Ai, kuthengo, kucipululu kumene anawapitikitsira, natha onse kugwa ndi lupanga lakuthwa mpaka adathedwa onse, Aisrayeli onse anabwerera ku Ai, naukantha ndi lupanga lakuthwa.

25 Ndipo onse amene adagwa tsiku lija, amuna ndi akazi, ndiwo zikwi khumi ndi ziwiri, anthu onse a ku Ai.

26 Popeza Yoswa sanabweza dzanja lace limene anatambasula nalo nthungo, mpaka ataononga konse nzika zonse za ku Ai.

27 Koma ng'ombe ndi zofunkha za mudzi uwu Israyeli anadzifunkhira monga mwa mau a Yehova amene analamulira Yoswa.

28 Ndipo Yoswa anatentha Ai, nausandutsa muunda ku nthawi yonse, bwinja kufikira lero lino.

29 Ndipo mfumu ya ku Ai, anampacika pamtengo mpaka madzulo; koma polowa dzuwa Yoswa analamulira kuti atsitse mtembo wace pamtengo; ndipo anauponya polowera pa cipata ca mudzi; nauniikako mulu waukuru wamiyala, mpaka lero lino.

30 Pomwepo Yoswa anamangira Yehova Mulungu wa Israyeli guwa la nsembe m'phiri la Ebala,

31 monga Mose mtumiki wa Mulungu adalamulira ana a Israyeli, monga mulembedwa m'buku la cilamulo ca Mose, guwa la nsembe la miyala yosasema, yoti palibe munthu anakwezapo citsulo; ndipo anafukizirapo Yehova nsembe zopsereza, naphera nsembe zoyamika.

32 Ndipo analembapo pa miyalayi citsanzo ca cilamulo ca Mose, cimene analembera pamaso pa ana a Israyeli.

33 Ndipo Aisrayeli onse, ndi akuru ao, ndi akapitao ao, ndi oweruza ao anaima cakuno ndi cauko ca likasa, pamaso pa ansembe Alevi, akusenza likasa la cipangano la Yehova, mbadwa ndi alendo omwe; ena a iwo pandunji pa phiri la Gerizimu, ndi ena pandunji pa phiri la Ebala; monga Mose, mtumiki wa Yehova, adalamulira poyamba pala kuti adalitse anthu a Israyeli,

34 Atatero, anawerenga mau onse a cilamulo, dalitso ndi temberero, monga mwa zonse zolembedwa m'buku la cilamulo.

35 Panalibe mau amodzi a zonse adazilamulira Mose osawerenga Yoswa pamaso pa msonkhano wonse wa Israyeli, ndi akazi ndi ang'ono, ndi alendo akuyenda pakati pao.

9

1 Yoswa anyengedwa ndi Agibeoni napangana nao. Ndipo kunali, pakumva ici mafumu onse a tsidya ilo la Yordano, kumapiri ndi kucidikha, ndi ku madoko onse a nyanja yaikuru, pandunji pa Lebano: Ahiti ndi Aamori, Akanani, Aperizi, Ahivi, ndi Ayebusi;

2 anasonkhana kuponyana ndi Yoswa ndi Israyeli, ndi mtima umodzi.

3 Koma pamene nzika za Gibeoni zinamva zimene Yoswa adacitira Yeriko ndi Ai,

4 zinacita momcenierera, nizimuka nizioneka ngati mithenga, nizitenga matumba akale pa aburu ao, ndi matumba a vinyo akale ndi ong'ambika ndi omangamanga;

5 ndi nsapato zakale za zigamba pa mapazi ao, nizibvala nsanza; ndi mikate yonse ya kamba wao inali youma ndi yoyanga nkhungu.

6 Ndipo zinamuka kwa Yoswa kumisasa ku Giligala, niziti kwa iye ndi kwa amuna a Israyeli, Tacokera dziko lakutali, cifukwa cace mupangane nafe.

7 Ndipo amuna a Israyeli anati kwa Ahivi, Kapena mulimkukhala pakati pa ife, ndipo tipanganenji ndi inu?

8 Koma anati kwa Yoswa, Ndife akapolo anu. Pamenepo Yoswa anati kwa iwo, Ndinu ayani? ndipo mufuma kuti

9 Ndipo anati kwa iye, Akapolo anu afumira dziko la kutalitali, cifukwa lea dzina la Yehova Mulungu wanu; pakuti tidamva mbiri yace, ndi zonse anacita m'Aigupto,

10 ndi zonse anacitira mafumu awiri a Aamori okhala tsidya lija la Yordano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni, ndi Ogi mfumu ya ku Basana wokhala ku Asitorotu.

11 Ndipo akuru athu ndi nzika zonse za m'dziko mwathu zidanena nafe ndi kuti, Mutenge m'dzanja lanu kamba wa paulendo, kakomane naoni, nimunene nao, Ndife akapolo anu; ndipo tsopano mupangane nafe.

12 Mkate wathu uwu tinadzitengera kamba m'nyumba zathu, ukali wamoto, tsiku loturuka Ife kudza kwanu kuno; koma tsopano, taonani, uli wouma ndi woyaoga nkhungu;

13 ndi matumba a vinyo awa tinawadzaza akali atsopano; ndipo taonani, ang'ambika; ndi malaya athu awa ndi nsapato zathu zatha, cifukwa ca ulendo wocokera kutali ndithu.

14 Pamenepo amunawo analandirako kamba wao, osafunsira pakamwa pa Yehova.

15 Ndipo Yoswa anacitirana nao mtendere, napangana nao, akhale amoyo; ndi akalonga a msonkhano anawalumbirira,

16 Ndipo kunali, atatha kupangana nao masiku atatu, anamva kuti ndiwo anansi ao, ndi kuti kwao ndi pakati pao,

17 Ndipo ana a Israyeli anayenda ulendo, nafika ku midzi yap tsiku lacitatu. Koma midzi yao ndiyo Gibeoni, ndi Cefira, ndi Beerotu ndi KiriyatuYearimu.

18 Ndipo ana a Israyeli sanawakantha, pakuti akalonga a msonkhano adawalumbirira kwa Yehova, Mulungu wa Israyeli. Ndipo msonkhano wonse unadandaula pa akalonga,

19 Koma akalonga onse ananena kwa msonkhano wonse, Tinawalumbirira kwa Yehova Mulungu wa Israyeli, m'mwemo sitikhoza kuwacitira kanthu.

20 Tidzawacitira ici, ndi kuwasunga amoyo; ungatigwere mkwiyo cifukwa ca lumbirolo tidawalumbirira.

21 Ndipo akalonga ananena nao, Akhale ndi moyo; ndipo anasanduka akutema nkhuni, ndi otungira madzi msonkhano wonse; monga akalonga adanena nao.

22 Ndipo Yoswa anawaitana, nanena nao, kuti, Mwatinyenga cifukwa ninji, ndi kuti, Tikhala kutaritari ndi inu, pokhala kwanu kuli pakati pa ife?

23 Ndipo tsopano mukhale otembereredwa, palibe mmodzi wa inu adzamasuka wosakhala kapolo, ndi kutemera nkhuni, ndi kutungira madzi nyumba ya Mulungu wanga.

24 Ndipo anamyankha Yoswa nati, Popeza anatiuzitsa akapolo anu kuti Yehova Mulungu wanu analamulira mtumiki wace Mose kukupatsani dziko lonseli, ndi kupasula nzika zonse za m'dziko pamaso panu; potero tinaopera kwambiri moyo wathu pamaso panu, ndipo tinacita cinthuci.

25 Ndipo tsopano, taonani, tiri m'dzanja lanu; monga muyesa cokoma ndi coyenera kuticitira ife, citani.

26 Pamenepo anawacitira cotero, nawalanditsa m'dzanja la ana a Israyeli, angawaphe.

27 Ndipo tsiku lija Yoswa anawasandutsa akutema nkhuni, ndi otungira madzi msonkhanowo, ndi guwa la nsembe la Yehova, mpaka lero lino, pamalopo akadzasankha.

10

1 Ndipo kunali, pamene Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu anamva kuti Yoswa adalanda Ai, ndi kumuononga konse; nacitira Ai ndi mfumu yace monga adacitira Yeriko ndi mfumu yace; ndi kuti nzika za Gibeoni zinacitirana mtendere ndi Israyeli, nizikhala pakati pao;

2 anaopa kwambiri, popeza Gibeoni ndi mudzi waukuru, monga wina wa midzi yacifumu, popezanso unaposa Ai kukula kwace, ndi amuna ace onse ndiwo amphamvu.

3 Cifukwa cace Adoni-Zedeki anatuma kwa Hohamu, mfumu ya Hebroni, ndi kwa Piraniu mfumu ya Yarimutu, ndi kwa Yafiya mfumu ya Lakisi, ndi kwa Dibri mfumu va Egiloni, ndi kuti,

4 Kwerani kwanga kuno, ndi kundithandiza kuti tikanthe Gibeoni, pakuti unacitirana mtendere ndi Yoswa ndi ana a Israyeli.

5 Pamenepo mafumu asanu a Aamori, ndiwo mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimutu, mfumu ya ku Lakisi, mfumu ya ku Egiloni anasonkhana, nakwera iwo ndi makamu ao onse namanga misasa pa Gibeoni, nauthira nkhondo.

6 Ndipo amuna a ku Gibeoni anatumira Yoswa mau kucigono ku Giligala, ndi kuti, Musalekerere akapolo anu; mutikwerere msanga, ndi kutipulumutsa, ndi kutithandiza; pakuti mafumu onse a Aamori, akukhala kumapiri atisonkhanira.

7 Pamenepo Yoswa anakwera kucokera ku Giligala, iye ndi anthu onse a nkhondo pamodzi naye, ndi ngwazi yose.

8 Ndipo Yehova ananena ndi Yoswa, Usawaope, pakuti ndawapereka m'dzanja lako; palibe mmodzi wa iwo adzaima pamaso pako.

9 Ndipo Yoswa anawadzidzimukitsa; popeza anakwera kucokera ku Giligala usiku wonse.

10 Ndipo Yehova anawamwaza pamaso pa Israyeli, ndipo anawakantha makanthidwe akuru ku Gibeoni, nawapitikitsa pa njira yokwera ya Betihoroni, nawakantha mpaka Azeka, ndi mpaka Makeda.

11 Ndipo kunali, pakuthawa iwo pamaso pa Israyeli, potsikira pa Betihoroni, Yehova anawagwetsera miyala yaikuru yocokera kumwamba mpaka pa Azeka, nafa iwo; akufa ndi miyala yamatalala anacuruka ndi iwo amene ana a Israyeli anawapha ndi lupanga.

12 Pomwepo Yoswa ananena kwa Yehova tsiku limene Yehova anapereka Aamori pamaso pa ana a Israyeli; ndipo anati pamaso pa Israyeli, Dzuwa iwe, linda, pa Gibeoni, Ndi Mwezi iwe, m'cigwa ca Aialo.

13 Ndipo dzuwa linalinda, ndi mwezi unaima Mpaka anthu adabwezera cilango adani ao. Kodi ici sicilembedwa m'buku la Yasari? Ndipo dzuwa linakhala pakati pa thambo, losafulumira kulowa ngati tsiku lamphumphu.

14 Ndipo panalibe tsiku lotere kale lonse kapena m'tsogolomo, lakuti Yehova anamvera mau a munthu; pakuti Yehova anathirira Israyeli nkhondo.

15 Pamenepo Yoswa anabwerera, ndi Aisrayeli onse pamodzi naye, ku cigono ca ku Giligala.

16 Ndipo mafumu awa asanu anathawa, nabisala m'phanga la ku Makeda,

17 Ndipo anauza Yoswa ndi kuti, Mafumu asanuwa apezeka obisala m'phanga la ku Makeda.

18 Ndipo Yoswa anati, Kunkhunizirani miyala yaikuru kukamwa kwa phanga, ndi kuikapo anthu, awasunge;

19 koma inu musaime, pitikitsani adani anu, ndi kukantha a m'mbuyo mwao; musawalole alowe m'midzi mwao; pakuti Yehova Mulungu wanu anawapereka m'dzanja lanu.

20 Ndipo kunali, Yoswa ndi ana a Israyeli atatha kuwakantha, makanthidwe akurukuru mpaka atatha psiti, ndipo otsala a iwo atalowa m'midzi ya malinga,

21 anthu onse anabwerera kucigono kwa Yoswa pa Makeda ndi mtendere. Palibe munthu anacitira cipongwe mmodzi yense wa ana a Israyeli.

22 Pamenepo Yoswa anati, Tsegula pakamwa pa phanga ndi kunditurutsira m'phanga mafumu asanuwo.

23 Ndipo anatero, naturutsira m'phanga mafumu asanuwo, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimutu, mfumu ya ku Lakisi, mfumu ya ku Egiloni.

24 Ndipo kunali, ataturutsira Yoswa mafumu awa, Yoswa anaitana amuna onse a Israyeli, ndipo anati kwa akazembe a anthu a nkhondo amene anamuka naye, Yandikirani, pondani pa makosi a mafumu awa. Nayandikira iwo, naponda pa makosi ao.

25 Pamenepo Yoswa ananena nao, Musaope, musatenge nkhawa; khalani amphamvu, nimulimbike mtima; pakuti Yehova adzatero ndi adani: anu onse amene mugwirana nao: nkhondo.

26 Ndipo atatero, Yoswa anawakantha nawapha, nawapacika pa mitengo isanu; nalikupacikidwa pa mitengo mpaka madzulo.

27 Ndipo kunali, nthawi yakulowa dzuwa, Yoswa analamulira kuti awatsitse kumitengo; ndipo anawataya m'phanga m'mene adabisala; naika miyala yaikuru pakamwa pa phanga, mpaka lero lomwe lino.

28 Ndipo Yoswa anagwira Makeda tsiku lomwe lija ndi kuukantha ndi lupanga lakuthwa, ndi mfumu yace yom we; anawaononga konse, ndi amoyo onse anali m'mwemo, osasiyapo ndi mmodzi yense, nacitira mfumu ya ku Makeda monga anacitira mfumu ya ku Yeriko.

29 Pamenepo Yoswa ndi Aisrayeli onse naye anapitirira kucokera ku Makeda kumka ku Libina, nathira nkhondo pa Libina;

30 ndipo Yehova anapereka uwunso, ndi mfumu yace m'dzanja la Israyeli; ndipo anaukantha ndi lupanga lakuthwa, ndi amoyo onse anali m'mwemo, osasiyamo ndi mmodzi yense; namcitira mfumu yace monga anacitira mfumu ya ku Yeriko.

31 Ndipo Yoswa, ndi Aisrayeli onse naye, anapitirira kucokera ku Libina kumka ku Lakisi; namanga misasa, nathira nkhondo pa uwo;

32 napereka Yehova Lakisi m'dzanja la Israyeli, ndipo anaulanda tsiku laciwiri, naukantha ndi lupanga lakuthwa, ndi amoyo onse anali m'mwemo monga mwa zonse anacitira Libina.

33 Pamenepo Horamu mfumu ya Gezere anakwera kudzathandiza Lakisi; ndipo Yoswa anamkantha iye ndi anthu ace mpaka sanamsiyira ndi mmodzi yense.

34 Ndipo Yoswa, ndi Aisrayeli onse naye, anapitirira kucokera ku Lakisi mpaka ku Egiloni; namanga nrisasa, nathira nkhondo.

35 Naulanda tsiku lomwelo, naukantha ndi lupanga lakuthwa, nawaononga konse amoyo onse anali m'mwemo tsiku lomwelo, monga mwa zonse anacitira Lakisi.

36 Ndipo Yoswa ndi Aisrayeli onse naye anakwera kucokera ku Egiloni mpaka ku Hebroni, nauthira nkhondo;

37 naulanda, naukantha ndi lupanga lakuthwa, ndi mfumu yace ndi midzi yace yonse, ndi amoyo onse anali m'mwemo, osasiyapo ndi mmodzi yense, monga mwa zonse anacitira Egiloni; koma anauononga konse, ndi amoyo onse anali m'mwemo.

38 Pamenepo Yoswa, ndi Aisrayeli onse naye, anabwerera kudza ku Dibiri, nauthira nkhondo,

39 naulanda, ndi mfumu yace ndi midzi yace yonse; naikantha ndi lupanga lakuthwa, naononga konse amoyo onse anali m'mwemo; sanasiya ndi mmodzi yense; monga anacitira Hebroni momwemo anacitira Dibiri ndi mfumu yace, monganso anacitira Libina ndi mfumu yace.

40 Motero Yoswa anakantha dziko lonse, la kumapiri, la kumwela, la kucidikha, la kuzigwa, ndi mafumu ao onse; sanasiyapo ndi mmodzi yense; koma anaononga psiti zonse zampweya, monga Yehova Mulungu wa Israyeli adalamulira.

41 Ndipo Yoswa anawakantha kuyambira Kadesi-Barinea mpaka ku Gaza, ndi dziko lonse la Goseni mpaka ku Gibeoni.

42 Ndipo Yoswa anagwira mafwnu awa onse ndi dziko lao nthawi yomweyi; cifukwa Yehova Mulungu wa Israyeli anathirira Israyeli nkhondo.

43 Pamenepo Yoswa ndi Aisrayeli onse naye, anabwerera kucigono ku Giligala.

11

1 Ndipo kunali, pamene Yabini mfumu ya ku Hazoro anacimva, anatwna kwa Yabobu mfumu ya ku Madoni, ndi kwa mfumu ya ku Simironi, ndi kwa mfumu ya ku Akasafu,

2 ndi kwa mafwnu akukhala kumpoto kumapiri, ndi kucigwa kwumwela kwa Kineroto, ndi kucidikha, ndi ku mitunda ya Doro kwnadzulo;

3 kwa Akanani kwn'mawa ndi kumadzulo, ndi kwa Aamori ndi Ahiti, ndi Aperizi ndi Ayebusi kumapiri, ndi kwa Ahivi kunsi kwa Herimoni, m'dziko la Mizipa.

4 Ndipo anaturuka, iwo ndi makamu ao onse nao, anthu ambiri, kucuruka kwao ngati mcenga uli m'mphepete mwa nyanja; ndi akavalo ndi magareta ambirimbiri.

5 Ndipo mafwnu awa onse anasonkhana, nadza namanga pamodzi ku madzi a Meromu, kumthira Israyeli nkhondo.

6 Koma Yehova anati kwa Yoswa, Usaope cifukwa ca iwowa; pakuti mawa, dzuwa lino ndidzawapereka onse ophedwa pamaso pa Israyeli; uziwadula mitsindo akavalo ao, ndi kutentha agareta ao ndi moto.

7 Ndipo Yoswa, ndi anthu onse a nkhondo naye, anawadzera modzidzimutsa ku madzi a Meromu, nawagwera.

8 Ndipo Yehova anawapereka m'dzanja la Israyeli, ndipo anawakantha, nawapitikitsa mpaka ku Zidoni waukulu, ndi ku MiseripotuMaimu, ndi ku cigwa ca Mizepe kum'mawa; nawakantha mpaka sanawasiyira ndi mmodzi yense.

9 Ndipo Yoswa anawacitira monga Yehova adamuuza: nadula akavalo ao mitsindo, natentha magareta ao ndi moto.

10 Ndipo Yoswa anabwerera m'mbuyo nthawi imeneyi nalanda Hazori nakantha mfumu yace ndi lupanga; pakuti kale Hazori unali waukuru wa maufumu aja onse.

11 Ndipo anakantha amoyo onse anali m'mwemo, ndi lupanga lakuthwa, ndi kuwaononga konse, osasiyapo ndi mmodzi yense wakupuma mpweya; ndipo anatentha Hazori ndi moto.

12 Ndipo Yoswa analanda midzi yonse ya mafumu awa, ndi mafumu ao omwe nawakantha ndi lupanga lakuthwa, nawaononga konse; monga Mose mtumiki wa Yehova adalamulira.

13 Koma midzi yonse yomangidwa pa zitunda zao Israyeli sanaitentha, koma wa Hazori wokha; wnenewu Yoswa anautentha.

14 Ndi zofunkha zonse za midzi iyi ndi ng'ombe ana a Israyeli anadzifunkhira; koma anakantha ndi lupanga lakuthwa anthu onse mpaka adawaononga osasiyapo ndi mmodzi yense wopuma mpweya.

15 Monga Yehova adalamulira Mose mtumiki wace, momwemo Mose analamulira Yoswa; momwemonso anacita Yoswa; sanacotsapo mau amodzi pa zonse Yehova adalamulira Mose.

16 Motero Yoswa analanda dziko lonselo, la kumapiri, ndi la kumwera, ndi dziko lonse la Goseni, ndi dziko la kucidikha, ndi la kucigwa; ndi la kwnapiri la Israyeli, ndi la ku cidikha cace;

17 kuyambira phiri la Halaki lokwera kumka ku Seiri, mpaka Baala-gadi m'cigwa ca Lebano patsinde pa phiri la Herimoni; nagwira mafwnu ao onse, nawakantha, nawapha.

18 Yoswa anathira nkhondo mafwnu awa onse nthawi yaikuru.

19 Palibe mudzi wakupangana mtendere ndi ana a Israyeli, koma Ahivi okhala m'Gibeoni; anaigwira yonse ndi nkhondo.

20 Pakuti cidadzera kwa Yehova kulimbitsa mitima yao kuti athirane nao Aisrayeli nkhondo kuti iye awaononge konse, kuti asawacitire cifundo koma awaononge, monga Yehova adalamulira Mose.

21 Ndipo Yoswa anadza nthawi yomweyo, napasula Aanaki kuwacotsa kumapiri, ku Hebroni, ku Dibiri, ku Anabi, ndi ku mapiri onse a Yuda, ndi ku mapiri onse a Israyeli; Yoswa anawaononga konse, ndi midzi yao yomwe.

22 Panalibe Aanaki otsala m'dziko la ana a Israyeli; koma m'Gaza, ndi m'Gati ndi m'Asidodo anatsalamo ena.

23 Motero Yoswa analanda dziko lonse monga mwa zonse Yehova adazinena kwa Mose; ndipo Yoswa analipereka kwa Israyeli, likhale lao lao, pfuko liri lonse gawo lace. Ndipo dziko linapumula nkhondo.

12

1 Ndipo awa ndi mafumu a dzikolo amene ana a Israyeli anwakantha, nalanda dziko lao tsidya la Yordano kum'mawa, kuyambira cigwa ca Arimoni, mpaka phiri la Herimoni, ndi cidikha conse ca kum'mawa;

2 Sihoni mfumu ya Aaroori wokhala m'Hesiboni, wocita ufumu kuyambira ku Aroeri ndiwo m'mphepete mwa cigwa ca Arinoni, ndi pakati pa cigwa ndi pa Gileadi wogawika pakati, kufikira mtsinje wa Yaboki, ndiwo malire a ana a Amoni;

3 ndi pacidikha mpaka nyanja ya Kineroti kum'mawa, ndi mpaka nyanja ya kucidikha, ndiyo Nyanja ya Mcere kum'mawa, njira ya Beti-Yesimoti; ndi kumwela pansi pa matsikiro a Pisiga.

4 Nalandanso malire a Ogi mfumu ya Basana wotsala wa Arefai, wokhala ku Asitarotu ndi ku Edrei,

5 nacita ufumu m'phiri la Herimoni, ndi m'Saleka, ndi m'Basana lonse, mpaka malire a Agesuri, ndi a Maakati, ndi Gileadi wogawika pakati, malire a Sihoni mfumu ya ku Hesiboni.

6 Mose mtumiki wa Yehova ndi ana a Israyeli anawakantha; ndi Mose mtumiki wa Yehova analipereka kwa Arubeni, ndi Agadi ndi pfuko la Manase logawika pakati, likhale colowacao.

7 Ndipo awa ndi mafumu a dzikolo amene Yoswa ndi ana a Israyeli anawakantha tsidya lija la Yordano kumadzulo, kuyambira Baala-gadi m'cigwa ca Lebano mpaka phiri la Halaki lokwera kumka ku Seiri; ndipo Yoswa analipereka kwa mapfuko a Israyeli, likhale lao lao, monga mwa magawo ao;

8 kumapiri ndi kucigwa, ndi kucidikha, ndi kumatsikiro, ndi kucipululu, ndi kumwela: Ahiti, Aamori, ndi Akanani, Aperizi, Ahivi ndi Ayebusi:

9 mfumu ya ku Yeriko, imodzi; mfumu ya ku Ai, ndiwo m'mbali mwa Beteli, imodzi;

10 mfumu ya ku Yerusalemu, imodzi; mfumu ya ku Hebroni, imodzi; mfumu ya ku Yarimutu, imodzi;

11 mfumu ya ku Lakisi, imodzi;

12 mfumu ya ku Egiloni, imodzi; mfumu ya ku Gezere, imodzi;

13 mfumu ya ku Dibiri, imodzi; mfumu ya ku Gederi, imodzi;

14 mfumu ya ku Horima, imodzi; mfumu ya ku Haradi, imodzi;

15 mfumu ya ku Libina, imodzi; mfumu ya ku Adulamu, imodzi;

16 mfumu ya ku Makeda, imodzi; mfumu ya ku Beteli, imodzi;

17 mfumu ya ku Tapuwa, imodzi; mfumu ya ku Heferi, imodzi;

18 mfumu ya ku Afeki, imodzi; mfumu ya ku Lasaroni, imodzi;

19 mfumu ya ku Madoni, imodzi; mfumu ya ku Hazori, imodzi;

20 mfumu ya ku Simironi-meroni, imodzi; mfumu ya ku Akasafu, imodzi;

21 mfumu ya ku Taanaki, imodzi; mfumu ya ku Megido, imodzi;

22 mfumu ya ku Kadesi, imodzi; mfumu ya ku Yokineamu ku Karimeli, imodzi;

23 mfumuya ku Doro, mpaka ponyamuka pa Doro, imodzi; mfumu ya ku Goimu m'Giligala, imodzi;

24 mfumu ya ku Tiriza, imodzi. Mafumu awa onse ndiwo makumi atatu ndi imodzi.

13

1 Ndipo Yoswa anakalamba, wa zaka zambiri; ndipo Yehova ananena naye, Wakalamba, wa zaka zambiri, ndipo latsala dziko lalikurukuru, alilandire colowa cao,

2 Dziko lotsala ndilo: malire onse a Afilisti, ndi Agesuri onse,

3 kuyambira Sihoro wokhala cakuno ca Aigupto mpaka malire a Ekironu kumpoto, loyesedwa la Akanani; akalonga asanu a Afilisti, a ku Gaza, ndi a ku Asidodi, a ku Asekelo, a ku Giti, ndi a ku Ekiro, ndi Ahivi;

4 kumwela dziko lonse la Akanani, ndi Meara ndiwo wa Asidoni, mpaka ku Afeka, mpaka ku malire a Aaroori;

5 ndi dziko la Agebili, ndi Lebano lonse kum'mawa, kuyambira Baala-gadi pa tsinde la phiri la Herimoni, mpaka polowera pace pa Hamati;

6 nzika zonse za kumapiri kuyambira Lebano, mpaka Misirepotumaimu, Asidoni onse; ndidzawainga pamaso pa ana a Israyeli, koma limeneli uwagawire Aisrayeli, likhale colowa cao, monga ndinakulamulira.

7 Ndipo tsopano uwagawire mapfuko asanu ndi anai, ndi pfuko la Manase logawika pakati, dziko ili likhale colowa cao.

8 Pamodzi ndi iye Arubeni ndi Agadi analandira colowa cao, cimene Mose adawapatsa tsidya ilo la Yordano kum'mawa, monga Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa;

9 kuyambira pa Aroeri, wokhala m'mphepete mwa cigwa ca Arinoni, ndi mudzi uti pakati pa cigwa, ndi cidikha conse ca Medeba mpaka ku Diboni;

10 ndi midzi yonse ya Sihoni mfumu ya Aamori, wakucita ufumu m'Hesiboni, mpaka malire a ana a Amoni;

11 ndi Gileadi, ndi malire a Agesuri, ndi Amaakati, ndi phiri lonse la Herimoni, ndi Basana ionse mpaka ku Saleka;

12 ufumu wonse wa Ogi m'Basana, wakucita ufumu m'Asitarotu, ndi m'Edrei (yemweyo anatsala pa otsala a Arefai); pakuti Mose anakantha awa, nawainga.

13 Koma ana a Israyeli sanainga Agesuri kapena Amaakati; koma Gesuri, ndi Maakati amakhala pakati pa Israyeli, mpaka lero lino.

14 Koma pfuko la Levi sanalipatsa colowa; nsembe za Yehova Mulungu wa Israyeli, zocitika ndi moto, ndizo colowa cace, monga iye adanena naye.

15 Ndipo Mose anapatsira pfuko la ana a Rubeni monga mwa mabanja ao.

16 Malire ao anayambira ku Aroeri wokhala m'mphepete mwa cigwa ca Arinoni, ndi mudzi uli pakati pa cigwa ndi cidikha conse ca ku Medeba;

17 Hesiboni ndi midzi yace yonse yokhala pacidikha; Diboni, ndi Bamoto-baala ndi Betibaala-Meoni;

18 ndi Yahaza ndi Kedemotu, ndi Mefaata;

19 ndi Kinyataimu, ndi Sibima, ndi Zeretisahara, m'phiri la kucigwa;

20 ndi Beti-peori, ndi matsikiro a Pisiga, ndi Beti-yesimotu;

21 ndi midzi yonse ya kucidikha, ndi ufumu wonse wa Sihoni mfumu ya Aamori, wocita ufumu m'Hesiboni, amene Mose anamkantha pamodzi ndi akalonga a Midyani, Evi, ndi Rekemu, ndi Zuri, ndi Huri ndi Reba, akalonga a Sihoni, nzika za m'dziko.

22 Ana a Israyeli anaphanso ndi lupanga Balamu mwana wa Beori, mlauli uja, pamodzi ndi ena adawaphawo.

23 Ndipo malire a ana a Rubeni ndiwo Yordano ndi malire ace. Ndico colandira ca ana a Rubeni monga mwa mabanja ao, midzi yace ndi miraga yace.

24 Ndipo Mose anapatsira pfuko la Gadi, ana a Gadi, monga mwa mabanja ao.

25 Ndipo malire ao ndiwo Yazeri, ndi midzi yonse ya Gileadi, ndi dziko la ana a Amoni logawika pakati, mpaka ku Aroeri, wokhala cakuno ca Raba;

26 ndi kuyambira Hesiboni mpaka Ramati-Mizipe, ndi Betonimu; ndi kuyambira Mahanaimu mpaka malire a Dibiri;

27 ndipo m'cigwa Betiharamu, ndi Beti-nimra, ndi Sukoti, ndi Zafoni, cotsala ca ufumu wa Sihoni mfumu ya Hesiboni, Yoidano ndi malire ace, mpaka malekezero a nyanja ya Kinereti, tsidya lija la Yordano kum'mawa.

28 Ici ndi colowa ca ana a Gadi, monga mwa mabanja ao, midzi yace ndi miraga yace.

29 Mose anaperekanso colowa kwa pfuko la Manase logawika pakati, ndico ca pfuko la Manase logawika pakati monga mwa mabanja ao.

30 Ndipo malire ao anayambira ku Mahanaimu, Basana lonse, ufumu wonse wa Ogi mfumu ya ku Basana, ndi midzi yonse ya Yairi, yokhala m'Basana, midzi makumi asanu ndi limodzi;

31 ndi Gileadi logawika pakati, ndi Asitarotu ndi Edrei, midzi ya ufumu wa Ogi m'Basana, inali ya ana a Makiri mwana wa Manase, ndiwo ana a Makiri ogawika pakati, monga mwa mabanja ao.

32 Izi ndi zolowazi Mose anazigawira m'zidikha za Moabu, tsidya ilo la Yordano ku Yeriko, kum'mawa.

33 Koma pfuko la Levi, Mose analibe kulipatsa colowa: Yehova Mulungu wa lsrayeli, ndiye colowa cao, monga ananena nao.

14

1 Ndipo awa ndi maiko ana a Israyeli anawalanda m'dziko la Kanani, amene Eleazare wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni, ndi akulu a nyumba za atate a mapfuko a ana a Israyeli, anawagawira.

2 Kulandira kwao kunacitika ndi kulota maere, monga Yehova adalamulira mwa dzanja la Mose, kunena za mapfuko asanu ndi anai ndi pfuko logawika pakati.

3 Pakuti Mose adapatsa mapfuko awiri, ndi pfuko logawika pakati, colowa tsidya ito la Yordano; koma sanapatsa Alevi colowa pakati pao,

4 Pakuti ana a Yosefe ndiwo mapfuko awiri, Manase ndi Efraimu; ndipo sanawagawira Alevi kanthu m'dziko, koma midzi yokhalamo ndi dziko lozungulirako likhale la zoweta zao ndi cuma cao.

5 Monga Yehova analamulira Mose, momwemo ana a Israyeli anacita, nagawana dziko.

6 Pamenepo ana a Yuda anadza kwa Yoswa ku Giligala; ndi Kalebe mwana wa Yefune Mkenizi ananena naye, Mudziwa cimene Yehova adanena kwa Mose munthu wa Mulungu za ine ndi za inu m'KadesiBarinea.

7 Ndinali ine wa zaka makumi anai muja Mose mtumiki wa Yehova anandituma kucokera ku Kadesi-Barinea, kukazonda dziko; ndipo ndinambwezera mau, monga momwe anakhala mumtima mwanga.

8 Koma abale anga amene anakwera nane anasungunutsa mitima ya anthu; koma ine ndinamtsata Yehova Mulungu wanga ndi mtima wanga wonse.

9 Ndipo Mose analumbira tsiku lomwelo ndi kuti, Zedi, dzikoli phazi lako lapondapo lidzakhala colowa cako, ndi ca ana ako kosalekeza, cifukwa unatsata Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse.

10 Ndipo tsopano, taonani, Yehova anandisunga ndi moyo, monga ananena, zaka izi mak umi anai ndi zisanu kuyambira nthawi ija Yehova ananena kwa Mose mau awa, poyenda Israyeli m'cipululu; ndipo tsopano taonani, ndine wa zaka makumi asanu ndi atatu, kudza zisanu lero lino.

11 Koma lero lino ndiri wamphamvu monga tsiku lija anandituma Mose; monga mphamvu yanga pamene paja, momwemo mphamvu yanga tsopano, kugwira nkhondo, ndi kuturuka ndi kulowa.

12 Ndipo tsopano, ndipatseni phiri ili limene Yehova ananenera tsiku lija; pakuti udamva tsiku lijalo kuti Aanaki anali komweko, ndi midzi yaikuru ndi yamalinga; kapena Yehova adzakhala ndi ine, kuti ndiwaingitse monga ananena Yehova.

13 Pamenepo Yoswa anamdalitsa, napatsa Kalebe mwana wa Yefune Hebroni likhale colowa cace.

14 Cifukwa cace Hebroni likhala colowa cace ca Kalebe mwana wa Yefune Mkenizi mpaka lero lino; popeza anatsata Yehova Mulungu wa Israyeli ndi mtima wonse.

15 Koma kale dzina la Hebroni linali mudzi wa Ariba, ndiye munthu wamkuru pakati pa Aanaki. Ndipo dziko linapumula nkhondo.

15

1 Ndipo gawo la pfuko la ana a Yuda monga mwa mabanja ao linafikira malire a Edomu, ku cipululu ca Zini kumwera, ku malekezero a kumwera.

2 Ndi malire ao a kumwera, anayambira ku malekezero a Nyanja ya Mcere, ku nyondo yoloza kumwera;

3 naturuka kumwela kwa cikweza ca Akarabi, napitirira ku Zini, nakwera kumwera kwa Kadesi-Barinea, napitirira ku Hezironi, nakwera ku Adara, nazungulira ku Karika;

4 napitirira ku Azimoni, naturuka ku mtsinje wa Aigupto; ndi malekezero a malirewa anali ku Nyanja Yaikuru; awa ndi malire anu a kumwera.

5 Ndi malire a kum'mawa ndiwo Nyanja ya Mcere, mpaka mathiriro ace a Yordano. Ndi malire a kumpoto anayambira nyondo ya nyanja ku mathiriro a Yordano;

6 nakwera malire kumka ku Beti-hogila, napitirira kumpoto kwa Beti-araba; nakwera malire kumka ku mwala wa Bohani mwana wa Rubeni;

7 nakwera malire kumka ku Dibiri, kucokera ku cigwa ca Akori, ndi kumpoto kupenyera Giligala ndiko kundunji kwa cikweza ca Adumi, ndiko kumwela kwa mtsinje; napitirira malire kumka ku madzi a Enisemesi, ndi maturukiro ace anali ku Eni-rogeli;

8 nakwera malire kumka ku cigwa ca mwana wa Hinomu, kumbali kwa Ayebusi, kumwela, ndiko Yerusalemu; nakwera malire kumka kumwamba kwa phiri lokhala patsogolo pa cigwa ca Hinomu kumadzulo, ndilo ku mathero ace a cigwa ca Refai kumpoto,

9 Ndipo analemba malire kuyambira pamwamba pa phiri mpaka citsime ca madzi ca Nefitoa, naturukira malire ku midzi ya phiri la Efroni; ndipo analemba malire kumka ku Baala, ndiwo Kiriyati-Yearimu.

10 Ndipo malire anazungulira kuyambira ku Baala kumka kumadzulo, ku phiri la Seiri, napitirira kumbali kwa phiri la Yearimu kumpoto, ndilo Kesaloni, natsikira ku Beti-semesi, napitirira ku Timina;

11 naturuka malire kumka ku mbali ya Ekroni kumpoto; ndipo analemba malire kumka ku Sikeroni, napitirira ku phiri la Baala, naturuka ku Yabindi; ndipo maturukiro a malire anali kunyanja.

12 Ndi malire a kumadzulo anali ku Nyanja Yaikuru ndiwo malire ace. Awa ndi malire a ana a Yuda pozungulira monga mwa mabanja ao.

13 Koma Yoswa anampatsa Kalebe mwana wa Yefune gawo mwa ana a Yuda, monga Yehova adamlamulira, ndiwo mudzi wa Ariba, ndiye atate wa Anaki, ndiwo Hebroni.

14 Ndipo Kalebe anaingitsako ana amuna atatu a Anaki, ndiwo Sesai, ndi Ahimani, ndi Talimai, ana a Anaki.

15 Nakwera komweko kumka kwa nzika za Dibiri; koma kale dzina la Dibiri ndilo Kiriyati-Seferi.

16 Ndipo Kalebe anati, iye amene akantha Kiriyati-Seferi, naulanda, yemweyo ndidzampatsa Akisa mwana wanga akhale mkazi wace.

17 Ndipo Otiniyeli mwana wa Kenazi, mbale wace wa Kalebe, anaulanda; ndipo anampatsa Akisa mwana wace akhale mkazi wace.

18 Ndipo kunali, m'mene anamdzera, anamkangamiza mwamuna wace kuti apemphe atate wace ampatse munda; ndipo anatsika pa buru; pamenepo Kalebe ananena naye, Ufunanji?

19 Nati iye, Mundipatse dalitso; popeza mwandipatsa dziko la kumwela, ndipatseninso zitsime za madzi. Pamenepo anampatsa zitsime za kumtunda, ndi zitsime za kunsi.

20 Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Yuda monga mwa mabanja ao.

21 Ndipo midzi ya ku malekezero a pfuko la ana a Yuda ku malire a Edomu, kumwela ndiwo, Kabizeeli ndi Ederi, ndi Yaguri;

22 ndi Kina ndi Dimona, ndi Adada;

23 ndi Kedesi, ndi Hazori, ndi ltinani;

24 Zifi ndi Telemu ndi Bealoti;

25 ndi Hazorihadata, ndi Kerioti-hezirondi, ndiwo Hazori;

26 Amamu ndi Sema ndi Moloda;

27 ndi Hazara-gada, ndi Hesimoni, ndi Beti-peleti;

28 ndi Hazara-suala, ndi Beereseba, ndi Bizioti;

29 Baala, ndi lyimu, ndi Ezemu;

30 ndi Elitoladi, ndi Kesili ndi Horima;

31 ndi Zikilaga, ndi Madimana ndi Sanasana;

32 ndi Lebaoti, ndi Siliimu, ndi Aini ndi Rimoni; midzi yonse ndiyo makumi awiri kudza isanu ndi inai; pamodzi ndi miraga yao.

33 Ku cigwa, Esitaoli, ndi Zora ndi Asina;

34 ndi Zoona, ndi Eniganimu, Tapua, ndi Enamu;

35 Yarimutu, ndi Adulamu, Soko, ndi Azeka;

36 ndi Saaraimu, ndi Aditaimu, ndi Gedera, ndi Gederotaimu; midzi khumi ndi inai pamodzi ndi miraga yao.

37 Zenani, ndi Hadasa, ndi Migidala-gadi;

38 ndi Dilani, ndi Mizipe, ndi Yokiteeli;

39 Lakisi ndi Bozikatu ndi Egiloni;

40 ndi Kaboni, ndi Lamasi, ndi, Kitilisi;

41 ndi Gaderotu, Beti-dagoni, ndi Naama, ndi Makeda; midzi khumi ndi isanu ndi umodzi pamodzi ndi miraga yao.

42 Libina ndi Eteri ndi Asana;

43 ndi Ifita ndi Asina ndi Nezibi;

44 ndi Kehila ndi Akisibu, ndi Maresa; midzi isanu ndi inai pamodzi ndi miraga yao.

45 Ekroni pamodzi ndi midzi yace ndi miraga yao;

46 kuyambira ku Ekroni mpaka kunyanja, yonse ya ku mbali ya Asidodo, pamodzi ndi miraga yao.

47 Asidodo, midzi yace ndi miraga yace; Gaza, midzi yace ndi miraga yace; mpaka mtsinje wa Aigupto, ndi nyanja yaikuru ndi malire ace.

48 Ndi kumapiri Samiri, ndi Yatiri, om Soko;

49 ndi Dana, ndi Kiriyatisana, ndiwo Dibiri;

50 ndi Anabi, ndi Esitemo, ndi Animu;

51 ndi Goseni, ndi Holoni, ndi Gilo; midzi khumi ndi umodzi pamodzi ndi miraga yao.

52 Arabu, ndi Duma, ndi Esana;

53 ndi Yanimu, ndi Beti-tapua, ndi Apeka;

54 ndi Humita, ndi Kiriyatiariba, ndiwo Hebroni, ndi Ziori; midzi isanu ndi inai pamodzi ndi miraga yao.

55 Maoni, Karimeli, ndi Zifu, ndi Yuta;

56 ndi Yesireeli, ndi Yokideamu, ndi Zoona;

57 Kaini, Gibea ndi Timina; midzi khumi pamodzi ndi miraga yao.

58 Haluli, Beti-zuru, ndi Gedori,

59 ndi Maaratu, ndi Bete-anotu, ndi Elitekoni; midzi isanu ndi umodzi pamodzi ndi miraga yao.

60 Kiriyata-Baala, ndiwo KiriyatiYearimu ndi Raba; midzi iwiri pamodzi ndi miraga yao.

61 M'cipululu, Beti-araba, Midini, ndi Sekaka;

62 ndi Nibisani, ndi Mudzi wa Mcere, ndi En-gedi; midzi isanu ndi umodzi pamodzi ndi miraga yao.

63 Koma ana a Yuda sanakhoza kuingitsa Ayebusi, nzika za Yerusalemu: m'mwemo Ayebusi anakhala pamodzi ndi ana a Yuda, ku Yerusalemu, mpaka lero lino.

16

1 Ndipo gawo La ana a Yosefe linaturuka kucokera ku Yordano ku Yeriko, ku madzi a Yeriko kum'mawa, kucipululu, nakwera kucokera ku Yeriko kumka kumapiri ku Beteli;

2 naturuka ku Beteli kumka ku Luzi, napitirira kumka ku malire a Aariki, ku Atarotu;

3 natsikira kumadzulo kumka ku malire a Ayafeleti, ku malire a Beti-horoni wa kunsi, ndi ku Gezeri; ndi maturukiro ace anali kunyanja.

4 Motero ana a Yosefe, Manase ndi Efraimu analandira colowa cao,

5 Ndipo malire a ana a Efraimu, monga mwa mabanja ao, ndiwo: malire a colowa cao kum'mawa ndiwo Atarotu-Adara, mpaka Betihoroni wa kumtunda;

6 naturuka malire kumadzulo ku Mikametatu kumpoto; nazungulira malire kum'mawa kumka ku Taanatu-silo, naupitirira kum'mawa kwace kwa Yanoa:

7 natsika kucokera ku Yanoa, kumka ku Atarotu, ndi ku Naara, nafika ku Yeriko, naturuka ku Yordano.

8 Kuyambira ku Tapua malire anamuka kumadzulo ku mtsinje wa Kana; ndi maturukiro ace anali kunyanja. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Efraimu monga mwa mabanja ao;

9 pamodzi ndi midzi adaipatulira ana a Efraimu pakati pa colowa ca ana a Manase, midzi yonse pamodzi ndi miraga yao.

10 Ndipo a sanaingitsa Akanani akukhala m'Gezeri; koma Akanani anakhala pakati pa Efraimu, kufikira lero lino, nawasonkhera msonkho.

17

1 Gawo la pfuko la Manase ndi ili: pakuti anali woyamba wa Yosefe. Makiri mwana woyamba wa Manase, atate wa Gileadi, popeza ndiye munthu wa nkhondo, anakhala nayo Gileadi ndi Basana.

2 Ndipo maere anagwera ana ena otsala a Manase monga mwa mabanja ao; ana a Abiezere ndi ana a Heleki, ndi ana a Asiriyeli, ndi ana a Sekemu ndi ana a Hefere, ndi ana a Semida; awa ndi ana amuna a Manase mwana wa Yosefe, monga mwa mabanja ao.

3 Koma Tselofekadi, mwana wa Hefere, mwana wa Gileadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase, analibe ana amuna koma ana akazi ndiwo; ndipo maina a ana ace akazi ndiwo: Mala, ndi Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.

4 Ndipo anayandikira pamaso pa Eleazare wansembe, ndi pamaso pa Yoswa mwana wa Nuni, ndi pamaso pa akalonga, ndi kuti, Yehova analamulira Mose atipatse colowa pakati pa abale athu; cifukwa cace anawapatsa monga mwa lamulo La Yehova, colowa pakati pa abale a atate wao.

5 Ndipo anamgwera Manase magawo khumi, osawerenga dziko la Gileadi ndi Basana lokhala tsidya lija la Yordano:

6 popeza ana akazi a Manase adalandira colowa pakati pa ana ace amuna; ndi dziko la Gileadi linakhala la ana a Manase otsala.

7 Ndipo malire a Manase anayambira ku Aseri, kumka ku Mika-metatu, wokhala cakuno ca Sekemu; namuka malire ku dzanja lamanja kwa nzika za Enitapua.

8 Dziko la Tapua linali la Manase; koma Tapua mpaka malire a Manase linakhala la ana a Efraimu.

9 Natsikira malire ku mtsinje wa Kana, kumwera kwa mtsinje; midzi iyi inakhala ya Efraimu pakati pa midzi ya Manase; ndi malire a Manase anali kumpoto kwa mtsinje; ndimaturukiro ace anali kunyanja;

10 kumwera nkwa Efraimu ndi kumpoto nkwa Manase, ndi malire ace ndi nyanja; ndi kumpoto anakomana ndi Aseri, ndi kum'mawa anakomana ndi Isakara.

11 Ndipo m'Isakara ndi m'Aseri Manase anali nao Betiseani ndi midzi yace, ndi Ibleamu ndi midzi yace, ndi nzika za Doro ndi midzi yace, ndi nzika za Eni-doro ndi midzi yace, ndi nzika za Taanaki ndi midzi yace, ndi nzika za Megido ndi midzi yace; dziko la mapiri atatu.

12 Koma ana a Manase sanatha kuingitsa a m'midzi aja, popeza Akananjanafuna kukhala m'dziko lija.

13 Ndipo kunali pamene ana a lsrayeli atakula mphamvu anasonkhetsa Akanani osawaingitsa onse.

14 Pamenepo ana a Yosefe ananena ndi Yoswa, ndi kuti, Watipatsiranji colowa cathu camaere cimodzi ndi gawo limodzi, popeza ife ndife anthu aunyinji, pakuti Yehova anatidalitsa ndi pano pomwe?

15 Ndipo Yoswa ananena nao, Ngati muli anthu aunyinji, kwerani kuli mitengoko, ndi kudziswera minda m'dziko la Aperizi ndi la Arefai; akakuceperani malo ku phiri la Efraimu.

16 Ndipo ana a Yosefe anati, Kuphiriko sikudzatifikira; ndipo Akananionse akukhala m'dziko la cigwa ali nao magareta acitsulo, iwo akukhala m'Bete-Seani, ndi midzi yace ndi iwo omwe akukhala m'cigwa ca Yezereli.

17 Ndipo Yoswa ananena kwa iwo a m'nyumba ya Yosefe, kwa Efraimu ndi Manase, ndi kuti, Inu ndinu anthu aunyinji, muli nayo mphamvu yaikuru; simudzakhala nalo gawo limodzi lokha;

18 koma kuphiriko kudzakhala kwanu pakuti pangakhale mpa mitengo, mudzisweretu minda, ndi maturukiro ace adzakhala anu; pakuti mudzaingitsa Akanani angakhale ali nao magareta acitsulo, angakhale ali amphamvu.

18

1 Ndipo msonkhano wonse wa ana a Israyeli unasonkhana ku Silo, nuutsa komweko cihema cokomanako; ndipo dziko linawagoniera.

2 Ndipo anatsala mwa ana a Israyeli mapfuko asanu ndi awiri osawagawira colowa cao.

3 Ndipo Yoswa anati kwa ana a Israyeli, Mucedwa mpaka liti kulowa ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu anakupatsani?

4 Mudzifunire amuna, pfuko liri lonse amuna atatu; kuti ndiwatume, anyamuke, nayendeyende iwo pakati pa dziko, nalilembe monga mwa colowa cao; nabwereoso kwa ine.

5 Ndipo adzaligawa magawo asanu ndi awiri; Yuda adzakhala m'malire ace kumwela, ndi a m'nyumba ya Yosefe adzakhala m'malire mwao kumpoto.

6 Ndipo muzilemba dziko likhale magawo asanu ndi awiri, ndi kubwera nao kuno kwa ine malembo ace; ndipo ndidzakuloterani maere pane pamaso pa Yehova Mulungu wathu.

7 Pakuti Alevi alibe gawo pakati pa inu; pakuti unsembe wa Yehova ndiwo colowa cao. Koma Gadi, ndi Rubeni, ndi pfuko la Manase logawika pakati adalandira colowa cao tsidya lija la Yordano kum'mawa, cimene Mose mtumiki wa Yehova adawapatsa.

8 Ndipo amunawo ananyamuka, namuka; ndipo Yoswa analamulira opita kulemba dzikowo, ndi kuti, Mukani, muyendeyende pakati pa dziko, ndi kulilemba, oimubwerenso kwa ine, ndipo ndidzakuloterani maere pane pamaso pa Yehova pa Silo.

9 Namuka amunawo, napitapita pakati pa dziko, nalilemba m'buku, nayesa midzi yace, magawo asanu, nabwera kwa Yoswa ku cigono ku Silo.

10 Ndipo Yoswa anawalotera maere ku Silo pamaso pa Yehova; ndi apo Yoswa anawagawira ana a Israyeli dziko, monga mwa magawo ao.

11 Ndipo maere a ana a Benjamini anakwera monga mwa mabanja ao; ndi malire a gawo lao anaturuka pakati pa ana a Yuda ndi ana a Yosefe.

12 Ndipo malire ao a kumpoto anacokera ku Yordano; ndi malire anakwera ku mbali ya Yeriko kumpoto, nakwera pakati pa mapiri kumadzulo; ndi maturukiro ace anali ku cipululu ca Beti-aveni.

13 Ndipo malire anapitirirapo kumka ku Luzi, ku mbali ya Luzi, momwemo ndi Beteli, kumwela; ndi malire anatsikira kumka ku Atarotu-adara, ku phiri lokhala kumwela kwa Betihoroni wa kunsi.

14 Ndipo malire analembedwa nazungulira ku mbali ya kumadzulo kumka kumwela, kucokera ku phiri pokhala patsogolo pa Beti-horoni, kumwela kwace; ndi maturukiro ace anali ku Kiriyatibaala, womwewo ndi Kiriyati-Yearimu, mudzi wa ana a Yuda; ndiyo mbali ya kumadzulo.

15 Ndipo mbali ya kumwela inayambira polekezera Kiriyati-Yearimu; naturuka malire kumka kumadzulo, naturuka kumka ku citsime ca madzi a Nefitoa;

16 natsikira malire kumka polekezera phiri lokhala patsogolo pa cigwa ca mwana wa Hinomu, ndico ca m'cigwa ca Refai kumpoto; natsikira ku cigwa ca Hinomu, ku mbali ya Ayebusi kumwela, natsikira ku Enirogeli;

17 nalembedwa kumka kumpoto, naturuka ku Eni-semesi, naturuka ku Gelilotu, ndiwo pandunji pokwerera pa Adumi; natsikira ku mwala wa Bohani mwana wa Rubeni;

18 napitirira ku mbali ya pandunji pa Araba kumpoto, natsikira kumka ku Araba;

19 napitirira malire kumka ku mbali ya Beti-hogila kumpoto; ndi maturukiro ace a malire anali ku nyondo ya kumpoto ya Nyanja ya Mcere; pa kulekezera kwa kumwela kwa Yordano; ndiwo malire a kumwera.

20 Ndipo malireace mbali ya kum'mawa ndiwo Yordano, ndico colowa ca ana a Benjamini, kunena za malire ace pozungulira pace, monga mwa mabanja ao.

21 Koma midzi ya pfuko la ana a Benjamini monga mwa mabanja ao ndiyo Yeriko, ndi Beti-hogila, ndi Emekikozizi;

22 ndi Beti-araba, ndi Zemaraimu, ndi Beteli;

23 ndi Arimu ndi Para, ndi Ofira;

24 ndi Kefaraamoni, ndi Ofini, ndi Geba; midzi khumi ndi iwiri pamodzi ndi miraga yao;

25 Gibeoni ndi Rama, ndi Beeroti;

26 ndi Mizipe, ndi Kefira, ndi Moza;

27 ndi Rekemu, ndi Iripeeli ndi Tarala;

28 ndi Zela, Elefi, ndi Yebusi, womwewo ndi Yerusalemu, Gibeati ndi Kiriyati; midzi khumi ndi inai pamodzi ndi miraga yace, Ndico colowa ca ana a Benjamini monga mwa mabanja ao.

19

1 Ndipo maere aciwiri anamturukira Simeoni, pfuko la ana a Simeoni monga mwa mabanja ao; ndi colowa cao cinali pakati pa colowa ca ana a Yuda.

2 Ndipo anali naco colowa cao Beeri-seba, kapena Seba, ndi Molada;

3 ndi Hazarasuala, ndi Bala, ndi Ezemu;

4 ndi Elitoladi, ndi Betuli, ndi Horimu;

5 ndi Zikilaga, ndi Beti-malikabotu, ndi Hazari-susa:

6 ndi Beti-lebaotu, ndi Saruheni; midzi khumi ndi itatu ndi miraga yao;

7 Aini, Rimoni ndi Eteri ndi Asana; midzi inai ndi miraga yao;

8 ndi miraga yonse yozungulira midzi iyi mpaka Baalata-beeri ndiwo Rama kumwera. Ndico colowa ca pfuko la ana a Simeoni, monga mwa mabanja ao.

9 M'gawo la ana a Yuda muli colowa ca ana a Simeoni; popeza gawo la ana a Yuda linawacurukira; cifukwa cace ana a Simeoni anali naco colowa pakati pa colowa coo.

10 Ndipo maere acitatu anakwecera ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao; ndi malire a colowa cao anafikira ku Saridi;

11 nakwera malire ao kumka kumadzulo ndi ku Marala nafikira ku Dabeseti, nafikira ku mtsinje wa patsogolo pa Yokineamu;

12 ndi kucokera ku Saridi anazungulira kumka kum'mawa kumaturukira dzuwa, mpaka malire a Kisilotu-tabori; naturuka kumka ku Daberati, nakwera ku Yafia;

13 ndi pocoka pamenepo anapitirira kumka kum'mawa ku Gati-heferi, ku Etikazini; naturuka ku Remoni umene ulembedwa mpaka ku Nea,

14 nauzungulira malire kumpoto, kumka ku Hanatoni; ndi maturukiro ace anali ku cigwa ca Ifita-eli;

15 ndi Kata, ndi Nahalala ndi Simironi, ndi Idala ndi Betelehemu: midzi khumi ndi iwiri ndi miraga yao.

16 Ici ndi colowa ca ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.

17 Maere acinai anamturukira Isakara, kunena za ana a Isakara monga mwa mabanja ao.

18 Ndi malire ao anali ku Yezireeli, ndi Kesulotu, ndi Sunemu;

19 ndi Hafaraimu, ndi Sioni, ndi Anaharati;

20 ndi Rabiti ndi Kisioni, ndi Ebezi;

21 ndi Remeti ndi Eni-ganaimu ndi Eni-hada, ndi Beti-Pazezi;

22 ndi malire anafikira ku Tabori, ndi Sahazuma, ndi Betesemesi; ndi maturukiro a malire ao anali ku Yordano; midzi khumi ndi isanu ndi umodzi ndi miraga yao.

23 Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Isakara, monga mwa mabanja ao, midzi ndi miraga yao.

24 Ndipo maece acisanu analiturukira pfuko la ana a Aseri monga mwa mabanja ao.

25 Ndi malire ao ndiwo Helikati, ndi Hali, ndi Beteni ndi Akisafu;

26 ndi Alameleki, ndi Amadi, ndi Misali; nafikira ku Karimeli kumadzulo ndi ku Sihorilibinati;

27 nazungulira koturukira dzuwa ku Beti-dagoni, nafikira ku Zebuloni ndi ku cigwa ca Ifita-eli, kumpoto ku Beti-emeki, ndi Nehieli; naturukira ku Kabulu kulamanzere,

28 ndi Ebroni, ndi Rehobo, ndi Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni wamkuru;

29 nazungulira malice kumka ku Rama, ndi ku mudzi wa linga la Turo; nazungulira malire kumka ku Hosa; ndi maturukiro ace anali kunyanja, kucokera ku Hebeli mpaka ku Akizibu;

30 Uma womwe ndi Afeki, ndi Rehobo; midzi makumi awiri mphambu iwiri ndi miraga yao,

31 Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Aseri monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miragayao.

32 Maere acisanu ndi cimodzi anaturukira ana a Nafitali, ana a Nafitali monga mwa mabanja ao.

33 Ndipo malire ao anayambira ku Helefi, ku thundu wa ku Zaanani, ndi Adaminekebi, ndi Yabineeli, mpaka ku Lakumu; ndi maturukiro ace anali ku Yordano;

34 nazungulira malire kumka kumadzulo ku Azinotu-tabori, naturukira komweko kumka ku Hukoku; nafikira ku Zebuloni kumwera, nafikira ku Aseri kumadzulo, ndi ku Yuda pa Yordano kum'mawa.

35 Ndipo midzi yamalinga ndiyo Zidimu, Zeri, ndi Hamati, Rakati, ndi Kinereti;

36 ndi Adama, ndi Rama, ndi Hazori;

37 ndi Kedesi, ndi Edrei, ndi Eni-hazori;

38 ndi Ironi, ndi Migidala-eli, Horemu, ndi Betianati, ndi Beti-semesi; midzi khumi ndi isanu ndi inai, ndi miraga yao.

39 Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Nafitali, monga mwa mabanja ao, midzi ndi miraga yao.

40 Maere acisanu ndi ciwiri anaturukira pfuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao.

41 Ndipo malire a colowa cao anali Zora, ndi Esitaoli ndi Iri-semesi;

42 Saalabini, ndi Aijaloni ndi ltila;

43 ndi Eloni ndi Timna ndi Ekroni;

44 ndi Eliteke, ndi Gibetoni, ndi Baalati;

45 ndi Yehudi, ndi Bene-beraki, ndi Gatirimoni;

46 ndi Me-jarikoni, ndi Rakoni, ndi malire pandunji pajapo.

47 Koma malire a ana a Dani anaturuka kupitirira iwowa; pakuti ana a Dani anakwera nathira nkhondo ku Lesemu, naulanda naukantha ndi lupanga lakuthwa, naulandira, nakhala m'mwemo, naucha Lesemu, Dani; ndilo dzina la Dani atate wao.

48 Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Dani, monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.

49 Ndipo atatha kuligawa dziko likhale colowa cao monga mwa malire ace, ana a Israyeli anapatsa Yoswa mwana wa Nuni colowa pakati pao;

50 monga mwa lamulo la Yehova anampatsa mudzi umene anawapempha, ndiwo Timinatisera, ku mapiri a Efraimu; ndipo anamangamudziwonakhala m'mwemo.

51 Izi ndizo zolowa anazigawa Eleazare wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni, ndi akulu a nyumba za atate a mapfuko a ana a Israyeli, zikhale zao zao, ndi kulota maere ku Silo pamaso pa Yehova ku khomo la cihema cokomanako. Momwemo anatha kuligawa dziko.

20

1 Ndipo Yehova anati kwa Yoswa,

2 Nena ndi ana a Israyeli ndi kuti, Mudziikire midzi yopulumukirako, monga ndinanena kwa inu mwa dzanja la Mose,

3 kuti athawireko wakupha munthu osamupha dala, osadziwa; ndipo idzakhalira inu yopulumukirako, kumpulumuka wolipsa mwazi.

4 Munthu akathawira umodzi wa midzi iyi, aziima polowera pa cipata ca mudziwo, nafotokozere mlandu wace m'makutu a akuru a mudziwo; pamenepo azimlandira kumudzi kwao, ndi kumpatsa malo, kuti akhale pakati pao.

5 Ndipo akamlondola wolipsa mwazi, asampereke m'dzanja lace wakupha mnzaceyo; pakuti anakantha mnansi wace mosadziwa, osamuda kale.

6 Ndipo azikhala m'mudzimo mpaka adzaima pamaso pa msonkhano anene mlandu wace, mpaka atafa mkulu wansembe wa m'masiku omwewo; pamenepo wakupha mnzace azibwerera ndi kufika kumudzi kwace, ndi nyumba yace, kumudzi kumene adathawako.

7 Ndipo anapatula Kedesi m'Galileya ku mapiri a Nafitali, ndi Sekemu ku mapiri a Efraimu, ndi mudzi wa Ariba ndiwo Hebroni ku mapiri a Yuda.

8 Ndipo tsidya lija la Yordano kum'mawa kwa Yeriko, anaika Bezeri m'cipululu, kucidikha, wa pfuko la Rubeni, ndi Ramoti m'Gileadi wa ofuko la Gadi, ndi Golani m'Basana wa pfuko la Manase.

9 Iyi ndi midzi yoikidwira ana onse a Israyeli, ndi mlendo wakukhala pakati pao, kuti athawireko ali yense wakupha munthu, ndi kuti asafe ndi dzanja la wolipsa mwazi, asanaime pamaso pa msonkhano.

21

1 Pamenepo akuru a nyumba za atate a Alevi anayandikira kwa Eleazare wansembe, ndi kwa Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa akuru a nyumba za atate a mapfuko a ana a Israyeli;

2 nanena nao ku Silo m'dziko la Kanani, ndi kuti Yehova analamulira mwa dzanja la Mose kuti atipatse midzi yokhalamo ife, ndi mabusa a zoweta zathu.

3 Ndipo ana a Israyeli anapatsa Alevi, kutapa pa colowa cao, monga mwa lamulo la Yehova, midzi iyi ndi mabusa ao.

4 Ndipo maere anaturukira mabanja a Akohati; ndipo molota maere ana a Aroni wansembe, ndiwo Alevi, analandira motapa pa pfuko la Yuda, ndi pa pfuko la Simeoni, ndi pa pfuko la Benjamini, midzi khumi ndi itatu.

5 Ndipo ana otsala a Kohati analandira molota maere motapa pa mabanja a pfuko la Efraimu, ndi pa pfuko La Dani, ndi pa pfuko La Manase logawika pakati, midzi khumi.

6 Ndipo ana a Gerisoni analandira molota maere motapa pa mabanja a pfuko la Isakara, ndi pa pfuko la Aseri, ndi pa pfuko la Nafitali, ndi pa pfuko la Manase logawika pakati m'Basana, midzi khumi ndi itatu.

7 Ana a Merari, monga mwa mabanja ao, analandira motapa pa pfuko la Rubeni, ndi pa pfuko la Gadi, ndi pa pfuko la Zebuloni midzi khumi ndi iwiri.

8 Motero ana a Israyeli anapatsa Alevi midzi iyi ndi mabusa ao, molota maere, monga Yehova adalamulira mwa dzanja la Mose.

9 Ndipo anapatsa motapa pa pfuko la ana a Yuda, ndi pa pfuko la ana a Simeoni, midzi iyi yochulidwa maina ao;

10 kuti ikhale ya ana a Aroni a mabanja a Akohati, a ana a Levi, pakuti maere oyamba adaturukira iwowa.

11 Ndipo anawapatsa mudzi wa Ariba, ndiye atate wa Anoki, womwewo ndi Hebroni, ku mapiri a Yuda, ndi mabusa ace ozungulirapo.

12 Koma minda ya mudzi ndi miraga yace anapatsa Kalebe mwana wa Yefune, ikhale yace.

13 Ndipo kwa ana a Aroni wansembe anapatsa Hebroni ndi mabusa ace, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzace, ndi Libina ndi mabusa ace;

14 ndi Yatiri ndi mabusa ace, ndi Esitimoa ndi mabusa ace;

15 ndi Holoni ndi mabusa ace, ndi Debiri ndi mabusa ace;

16 ndi Aini ndi mabusa ace, ndi Yuta ndi mabusa ace, ndi Betisemesi ndi mabusa ace; midzi isanu ndi inai yotapira mapfuko awiri aja.

17 Ndipo motapira pfuko La Benjamini, Gibeoni ndi mabusa ace, Geba ndi mabusa ace,

18 Anatotu ndi mabusa ace, ndi Alimoni ndi mabusa ace; midzi inai.

19 Miclzi yonse ya ana a Aroni, ansembe, ndiyo khumi ndi itatu, ndi mabusa ao.

20 Ndipo mabanja a ana a Kohati, Aleviwo, otsala a ana a Kohati, analandira midzi ya maere ao motapira pa pfuko la Efraimu.

21 Ndipo anawapatsa Sekemu ndi mabusa ace ku mapiri a Efraimu, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo, ndi Gezeri ndi mabusa ace;

22 ndi Kibizaimu ndi mabusa ace, Betihoroni ndi mabusa ace; midzi inai.

23 Ndipo motapira m'pfuko La Dani, Eliteke ndi mabusa ace, Gibetoni ndi mabusa ace;

24 Aijaloni ndi mabusa ace, Gati-rimoni ndi mabusa ace; midzi inai.

25 Ndipo motapira pa pfukola Manaselogawika pakati, Taanaki ndi mabusa ace, ndi Gati-rimoni ndi mabusa ace; midzi iwiri.

26 Midzi yonse ya mabanja a ana otsala a Kohati ndiyo khumi ndi mabusa ao.

27 Ndipo anapatsa ana a Gerisoni, a mabanja a Alevi, motapira pa pfuko la Manase logawika pakati, Golani m'Basana ndi mabusa ace, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo; ndi Beesitera ndi mabusa ace; midzi iwiri.

28 Ndipo motapira pa pfuko la Isakara, Kisioni ndi mabusa ace, Daberati ndi mabusa ace;

29 Yarimutu ndi mabusa ace, Eniganimu ndi mabusa ace; midzi inai.

30 Ndipo motapira pa pfuko La Aseri, Misali ndi mabusa ace, Abidoni ndi mabusa ace;

31 Helikati ndi mabusa ace, ndi Rehobo ndi mabusa ace; midzi inai.

32 Ndipo motapira pa pfuko la Nafitali, Kedesi m'Galileya ndi mabusa ace, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo, ndi Hamotidori ndi mabusa ace, ndi Karitani ndi mabusa ace, midzi itatu.

33 Midzi yonse ya Agerisoni monga mwa mabanja ao ndiyo midzi khumi ndi itatu ndi mabusa ao.

34 Ndipo anapatsa kwa mabanja a ana a Merari, otsala a Alevi, motapira pa pfuko la Zebuloni, Yokineamu ndi mabusa ace, ndi Karita ndi mabusa ace,

35 Dimna ndi mabusa ace, Nahalala ndi mabusa ace; midzi inai.

36 Ndipo motapira pa pfuko la Rubeni, Bezeri ndi mabusa ace, ndi Yahazi ndi mabusa ace,

37 Kedimotu ndi mabusa ace, ndi Mefati ndi mabusa ace; midzi inai.

38 Ndipo motapira m'pfuko la Gadi, Ramoti m'Gileadi ndi mabusa ace ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo, ndi Mahanaimu ndi mabusa ace;

39 Hesiboni ndi mabusa ace. Yazeri ndi mabusa ace: yonse pamodzi midzi inai.

40 Yonseyi ndiyo midzi ya ana a Merari monga mwa mabanja ao, ndiwo otsala a mabanja a Alevi; ndipo gawo lao ndilo midzi khumi ndi iwiri.

41 Midzi yonse ya Alevi, pakati pa colowa ca ana a Israyeli ndiyo midzi makumi anai kudza isanu ndi itatu, ndi mabusa ao.

42 Midzi iyi yonse inali nao mabusa ao pozungulira pao: inatero midzi iyi yonse.

43 Motero Yehova anawapatsa Israyeli dziko lonse adalumbiralo kuwapatsa makolo ao: ndipo analilandira lao lao, nakhala m'mwemo.

44 Ndipo Yehova anawapatsa mpumulo pozungulira ponse, monga mwa zonse adalumbirira makolo ao; ndipo pamaso pao sipanaima munthu mmodzi wa adani ao onse; Yehova anapereka adani ao onse m'manja mwao.

45 Sikadasowa kanthu konse ka zinthu zokoma zonse Yehova adazinenera nyumba ya Israyeli; zidacitika zonse.

22

1 Pamenepo Yoswa anaitana Arubeni ndi Agadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati,

2 nanena nao, Mwasunga inu zonsezo anakulamulirani Mosemtumiki wa Yehova; mwamveranso mau anga m'zonse ndinakulamulirani inu;

3 simunasiya abale anu masiku awa ambiri mpaka lero lino, koma mwasunga cisungire lamulola Yehova Mulungu wanu.

4 Ndipo tsopano Yehova Mulungu wanu wapumitsa abale anu, monga adanena nao; potero bwererani tsopano, mu kani ku mahema anu, ku dziko la colowa canu cimene Mose mtumiki wa Yehova anakuninkhani tsidya lija la Yordano.

5 Koma samalirani bwino kuti mucite cilangizo ndi cilamulo zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulirani kukonda Yehova Mulungu wanu, ndi kuyenda m'njira zace zonse ndi kusunga malamulo ace, ndi kumuumirira iye, ndi kumtumikira iye ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.

6 Momwemo Yoswa anawadalitsa, nawauza amuke; ndipo anamuka ku mahema ao.

7 Ndipo gawo limodzi la pfuko la Manase, Mose anawapatsa colowa m'Basana; koma gawo lina Yoswa anawaninkha colowa pakati pa abale ao tsidya lija la Yordano kumadzulo. Ndiponso pamene Yoswa anawauza amuke ku mahema ao, anawadalitsa;

8 nanena nao ndi kuti, Bwererani naco cuma cambiri ku mahema anu, ndi zoweta zambirimbiri, ndi siliva, ndi golidi, ndi mkuwa, ndi citsulo, ndi maraya ambirimbiri; mugawane nao abale anu zofunkha kwa adani anu.

9 Ndipo ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati anabwerera, nacoka kwa ana a Israyeli ku Silo, ndiwo wa m'dziko la Kanani kumka ku dziko la Gileadi, ku dziko lao lao, limene anakhala eni ace, monga mwa lamulo la Yehova, mwa dzanja la Mose.

10 Ndipo pamene anafikira mbali ya ku Yordano, ndilo la m'dziko la Kanani, ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati anamanga ku Yordano guwa la nsembe, guwa lalikuru maonekedwe ace.

11 Ndipo ana a Israyeli anamva anthu akuti, Taonani ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati anamanga guwa la nsembe pandunji pa dziko la Kanani, ku mbali ya ku Yordano, ku mbali ya ana a Israyeli.

12 Pamene ana a Israyeli anamva ici msonkhano wonse wa ana a Israyeli anasonkhana ku Silo, kuti awakwerere kuwathira nkhondo.

13 Ndipo ana a Israyeli anatumiza kwa ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati, ku dziko la Gileadi, Pinehasi mwana wa Eleazare wansembe,

14 ndi akalonga khumi naye; nyumba imodzi ya atate kalonga mmodzi, kotero ndi mapfuko onse a Israyeli; yense wa iwowa ndiye mkuru wa nyumba ya atate ao mwa mabanja a Israyeli.

15 M'mene anafika kwa ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati, ku dziko la Gileadi, ananena nao ndi kuti,

16 Utero msonkhano wonse wa Yehova, Colakwa ici nciani mwalakwira naco Mulungu wa Israyeli, ndi kumtembenukira Yehova lero line kusamtsatanso, popeza munadzimangira guwa la nsembe kupikisana ndi Yehova lero lino?

17 Kodi mphulupulu ya ku Peori iticepera, imene sitinadziyeretsera mpaka lero lino, ungakhale mliri unadzera msonkhano wa Yehova,

18 kuti mubwerera lero line kusatsata Yehova? ndipo kudzakhala kuti popeza lero mupikisana ndi Yehova, mawa adzakwiyira msonkhano wonse wa Israyeli.

19 Koma mukayesa dziko La colowa canu ncodetsa, olokani kulowa m'dziko lacolowaca Yehova m'mene cihemaca Yehovacikhalamo, nimukhale naco colowa pakati pa ife; koma musapikisana ndi Yehova kapena kupikisana nafe, ndi kudzimangira nokha guwa la nsembe, pamodzi ndi guwa la nsembe la Yehova Mulungu wathu.

20 Kodi Akani mwana wa Zera sanalakwa m'coperekedwaco, ndipo mkwiyo unagwera msonkhano wonse wa Israyeli? osangoonongeka yekha munthuyo mu mphulupulu yace.

21 Pamenepo ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati anayankha, nanena ndi akuru a mabanja a Israyeli,

22 Yehova Cauta Mulungu, Yehova Cauta Mulungu, iye adziwa, ndi Israyeli adzadziwa; ngati mopikisana, ngati molakwira Yehova,

23 tadzimangira guwa la nsembe, kubwerera kusamtsata Yehova, musatipulumutsa lero lino; kapena ngati kufukizapo nsembe yopsereza, kapena nsembe yaufa, kapena kuperekapo nsembe zoyamika, acifunse Yehova mwini wace;

24 ndipo ngati ife sitinacita ici cifukwa ca kuopa mlandu, ndi kuti, Masiku akudzawo ana anu akadzanena ndi ana athu, ndi kuti, Muli ciani inu kwa Yehova Mulungu wa Israyeli?

25 pakuti Yehova anaika Yordano ukhale malire pakati pa ife ndi inu, ana a Rubeni, ndi ana a Gadi; mulibe gawo ndi Yehova; motero ana anu adzaleketsa ana athu asaope. Yehova.

26 Cifukwa cace tinati, Tiyeni tikonzeretu zotimangira guwa la nsembe, si kufukizapo nsembe yopsereza ai, kapena nsembe yophera ai;

27 koma lidzakhala mboni pakati pa ife ndi inu; ndi pakati pa mibadwo yathu ya m'tsogolo, kuti tikacita nchito ya Yehova pamaso pace ndi nsembe zathu zopsereza, ndi zophera, ndi zoyamika; kuti ana anu asanene ndi ana athu m'tsogolomo, Mulibe gawo ndi Yehova.

28 Cifukwa cace tinati, Kudzali, akadzatero kwa ife, kapena kwa mibadwo yathu m'tsogolomo, kuti tidzati, Tapenyani, citsanzo ca guwa la nsembe la Yehova, comanga makolo athu, si kufukizapo nsembe yopsereza ai, kapena nsembe yophera ai, koma ndilo mboni pakati pa ife ndi inu.

29 Sikungatheke kuti tipikisane ndi Yehova ndi kubwerera lero kusatsata Yehova, kumanga guwa la nsembe la kufukizapo nsembe yopsereza, la nsembe yaufa, kapena yophera, pamodzi ndi guwa la nsembe la Yehova Mulungu wathu lokhala pakhomo pa cihema cace.

30 Pamene Pinehasi wansembe, ndi akalonga a msonkhano ndi akuru a mabanja a Israyeli okhala naye anamva mau adawanena ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi ana a Manase, anawakomera pamaso pao.

31 Ndipo Pinehasi, mwana wa Eleazare wansembe ananena ndi ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi ana a Manase, Lero lino tidziwa kuti Yehova ali pakati pa ife, pakuti simunalakwira naco Yehova; tsopano mwalanditsa ana a Israyeli m'dzanja la Yehova.

32 Ndipo Pinehasi mwana wa Eleazare wansembe, ndi akalonga anabwerera kucokera kwa ana a Rubeni, ndi kwa ana a Gadi, m'dziko la Gileadi, kudza ku dziko La Kanani kwa ana a Israyeli, nawabwezera mau.

33 Ndipo mauwo anakomera ana a Israyeli pamaso pao; ndi ana a Israyeli analemekeza Mulungu, osanenanso za kuwakwerera ndi kuwathira nkhondo, kuliononga dziko lokhalamo ana a Rubeni ndi ana a Gadi.

34 Ndipo ana a Rubeni ndi: ana a Gadi analicha guwa la nsembelo: Ndilo mboni pakati pa ife kuti Yehova ndiye Mulungu.

23

1 Ndipo atapita masiku ambiri, Yehova atapumulitsa Israyeli kwa adani ao onse akuwazungulira, ndipo Yoswa adakalamba nakhala wa zaka zambiri;

2 Yoswa anaitana Aisrayeli onse, akulu akulu ao, ndi akuru ao, ndi oweruza ao, ndi akapitao ao, nanena nao, Ndakalamba, ndine wa zaka zambiri;

3 ndipo munapenya zonse Yehova Mulungu anacitira mitundu iyi yonse ya anthu cifukwa ca inu; pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anakuthirirani nkhondo.

4 Taonani, ndakugawirani mitundu ya anthu iyi yotsala ikhale colowa ca mapfuko anu, kuyambira ku Yordano, ndi mitundu yonse ya anthu ndinaipasula, mpaka ku nyanja yaikuru ku malowero a dzuwa.

5 Ndipo Yehova Mulungu wanu Iyeyu adzawapitikitsa pamaso panu, ndi kulanda dziko lao kuwacotsa pamaso panu, ndipo mudzalandira dziko lao likhale colowa canu; monga Yehova Mulungu wanu ananena ndi inu.

6 Koma mulimbike mtima kwambiri kusunga ndi kucita zonse zolembedwa m'buku la cilamulo ca Mose, osacipambukira kulamanja kapena kulamanzere;

7 osalowa pakati pa amitundu awa otsala mwa inu; kapena kuchula dzina la milungu yao; osalumbiritsa nalo, kapena kuitumikira, kapena kuigwadira;

8 koma muumirire Yehova Mulungu wanu, monga munacita mpaka lero lino.

9 Pakuti Yehova anaingitsa pamaso panu mitundu yaikuru ndi yamphamvu; koma inu, palibe munthu anaima pamaso panu mpaka lero lino.

10 Munthu mmodzi wa inu adzapitikitsa anthu cikwi cimodzi; pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye amathirira inu nkhondo monga ananena ndi inu.

11 Potero mudzisamalire ndithu kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.

12 Koma, mukadzabwereram'mbuyo pang'ono pokha ndi kuumirira otsala a mitundu awa, ndiwo akutsala pakati pa inu, ndi kukwatitsana nao, ndi kulowana nao, naonso kulowana nanu;

13 dziwani ndithu kuti Yehova Mulungu wanu sadzalandanso dziko la amitundu awa kuwacotsa pamaso panu; koma adzakhala kwa inu deka ndi msampha ndi mkwapulo m'nthiti mwanu, ndi minga m'maso mwanu, mpaka mudzatayika m'dziko lokoma ili anakupatsani Yehova Mulungu wanu.

14 Ndipo taonani, lero lino ndirikumuka njira ya dziko lonse lapansi; ndipo mudziwa m'mitima yanu yonse, ndi m'moyo mwa inu nonse, kuti pa mau okoma onse Yehova Mulungu wanu anawanena za inu sanagwa padera mau amodzi; onse anacitikira inu, sanasowapo mau amodzi.

15 Ndipo kudzakhala kuti monga zakugwerani zokoma zonse anakunenerani Yehova Mulungu wanu, momwemo Yehova adzakutengerani zoipa zonse mpaka atakuonongani kukucotsani m'dziko lokoma ili anakupatsani Yehova Mulungu wanu.

16 Mukalakwira cipangano ca Yehova Mulungu wanu cimene analamulira inu ndi kumuka ndi kutumikira milungu yina ndi kuigwadira, mkwiyo wa Mulungu udzayakira inu, nimudzatayika msanga m'dziko lokomali anakupatsani.

24

1 Ndipo Yoswa anasonkhanitsa mapfuko onse a Israyeli ku Sekemu, naitana akulu akulu a Israyeli ndi akuru ao, ndi oweruza ao, ndi akapitao ao; ndipo anadzilangiza pamaso pa Mulungu.

2 Ndipo Yoswa ananena ndi anthu onse, Atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Kale lija makolo anu anakhala tsidya lija la mtsinje, ndiye Tera, atate wa Abrahamu ndi atate wa Nahori; natumikira milungu yina iwowa.

3 Ndipo ndinamtenga kholo lanu Abrahamu tsidya lija la mtsinje, ndi kumuyendetsa m'dziko lonse la Kanani ndi kucurukitsa mbeu zace ndi kumpatsa Isake,

4 Ndi kwa Isake ndinapatsa Yakobo ndi Esau, ndipo ndinampatsa Esau phiri la Seiri likhale lace lace; koma Yakobo ndi ana ace anatsikira kumka ku Aigupto.

5 Pamenepo ndinatuma Mose ndi Aroni, ndipo ndinasautsa Aigupto, monga ndinacita pakati pace; ndipo nditatero ndinakuturutsani.

6 Ndipo ndinaturutsa atate anu m'Aigupto; ndipo munadzakunyanja; koma Aaigupto analondola atate anu ndi magareta ndi apakavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.

7 Ndipo pamene anapfuula kwa Yehova, anaika mdima pakati pa inu ndi Aaigupto nawatengera nyanja, nawamiza; ndi maso anu anapenya cocita Ine m'Aigupto; ndipo munakhala m'cipululu masiku ambiri.

8 Pamenepo ndinakulowetsani inu m'dziko la Aamori okhala tsidya lija la Yordano; nagwirana nanu iwowa; ndipo ndinawapereka m'dzanja lanu, nimunalandira dziko lao likhale lanu lanu; ndipo ndinawaononga pamaso panu.

9 Pamenepo Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Moabu, anauka naponyana ndi Israyeli; natuma naitana Balamu mwana wa Beori atemberere inu;

10 koma sindinafuna kumvera Balamu, potero anakudalitsani cidalitsire, ndipo ndinakulanelitsani m'dzanja lace.

11 Pamenepo munaoloka Yordano, ndi kufika ku Yeriko; ndi eni ace a ku Yeriko anaponyana nanu nkhondo, Aamori, ndi Aperizi, ndi Akanani, ndi Ahiti, ndi Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi; ndipo ndinawapereka m'dzanja lanu.

12 Ndipo ndinatuma mabvu atsogolere inu, amene anawaingitsa pamaso panu, ndiwo mafumu awiri a Aamori; osati ndi lupanga lako, kapena ndi uta wako ai.

13 Ndipo ndinakupatsani dziko limene simunagwiramo nchito, ndi midzi simunaimanga, ndipo mukhala m'mwemo; mukudya za m'minda yamphesa, ndi minda yaazitona imene simunaioka.

14 Ndipo tsopano, opani Yehova ndi kumtumikira ndi mtima wangwiro ndi woona; nimucotse milungu imene makolo anu anaitumikira tsidya lija la mtsinje, ndi m'Aigupto; nimutumikire Yehova.

15 Ndipo ngati kutumikira Yehova kukuipirani mudzisankhire lero amene mudzamtumikira, kapena milungu imene anaitumikira makolo anu okhala tsidya lija la mtsinje, kapena milungu ya Aamori amene mukhala m'dziko lao; koma ine, ndi a m'nyumba yanga, tidzatumikira Yehova.

16 Ndipo anthu anayankha, nati, Sikungatheke kuti timsiye Yehova, ndi kutumikira milungu yina;

17 pakuti Yehova Mulungu wathu ndi iye amene anatikweza kutiturutsa m'dziko la Aigupto ku nyumba ya akapolo, nacita zodabwiza zazikuruzo pamaso pathu, natisunga m'njira monse tidayendamo, ndi pakati pa anthu onse amene tinapita pakati pao;

18 ndipo Yehova anaingitsa pamaso pathu anthu awa onse, ngakhale Aamori okhala m'dzikomo; cifukwa cace ifenso tidzatumikira Yehova, pakuti ndiye Mulungu wathu.

19 Ndipo Yoswa anati kwa anthu, Simukhoza inu kutumikira Yehova pakuti ndiye Mulungu woyera, ndi Mulungu wansanje; sadzalekerera zolakwa zanu, kapena zocimwa zanu.

20 Mukasiya Yehova, ndi kutumikira milungu yacilendo, adzatembenuka ndi kukucitirani coipa, ndi kukuthani, angakhale anakucitirani cokoma.

21 Ndipo anthu anati kwa Yoswa, Iaitu, koma tidzatumikira Yehova.

22 Ndipo Yoswa ananena ndi anthu, Inu mwadzicitira mboni inu nokha kuti mwadzisankhira Yehova kumtumikira iye. Ndipo anati, Ndife mboni.

23 Ndipo tsopano, cotsani milungu yacilendo iri pakati pa inu, ndi kulozetsa mitima yanu kwa Yehova, Mulungu wa Israyeli.

24 Ndipo anthu anati kwa Yoswa, Tidzamtumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera mau ace.

25 Motero Yoswa anacita pangano ndi anthu tsiku lija, nawaikira lemba ndi ciweruzo m'Sekemu.

26 Ndipo Yoswa analembera mau awa m'buku la cilamulo ca Mulungu; natenga mwala waukuru, nauimitsa apo patsinde pa thundu wokhala pa malo opatulika a Yehova.

27 Ndipo Yoswa anati kwa anthu onse, Taonani, mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa; pakuti udamva mau onse a Yehova amene ananena kwa ife; ndipo udzakhala mboni yotsutsa inu, mungakanize Mulungu wanu.

28 Pamenepo Yoswa anauza anthu amuke, yense ku colowa cace.

29 Ndipo kunali, zitatha izi, Yoswa mwana wa Nuni mtumiki wa Yehova, adafa, wa zaka zana ndi khumi.

30 Ndipo anamuika m'malire a colowa cace m'Timinati-sera, ndiwo ku mapiri a Efraimu kumpoto kwa phiri la Gaasi.

31 Ndipo Israyeli anatumikira Yehova masiku onse a Yoswa, ndi masiku onse a akulu akulu otsala atafa Yoswa, amene anadziwa nchito yonse ya Yehova anaicitira Israyeli.

32 Ndipo mafupa a Yosefe amene ana a Israyeli anakwera nao kucokera ku Aigupto anawaika ku Sekemu, pa kadziko kamene adakagula Yakobo kwa ana a Hamori atate wa Sekemu ndi kuwapatsa ndalama zana; ndipo anakhala colowa ca ana a Yosefe.

33 Eleazarenso mwana wa Aroni anafa; ndipo anamuika pa phiri la Pinehasi mwana wace, limene adampatsa ku mapiri a Efraimu.