1

1 NDIPO Solomo mwana wa Davide analimbikitsidwa m'ufumu wace, ndipo Yehova Mulungu wace anali naye, namkuza kwakukuru.

2 Ndipo Solomo analankhula ndi Aisrayeli onse, ndi akuru a zikwi ndi a mazana, ndi kwa oweruza, ndi kwa kalonga ali yense wa Israyeli, akuru a nyumba za makolo.

3 Ndipo Solomo ndi khamu lonse pamodzi naye anamuka ku msanje wa ku Gibeoni; pakuti kumeneko kunali cihema cokomanako ca Mulungu adacimanga Mose mtumiki wa Yehova m'cipululu.

4 Koma likasa la Mulungu Davide adakwera nalo kucokera ku Kiriyati Yearimu kumka kumene Davide adalikonzeratu malo; pakuti adaliutsiratu hema ku Yerusalemu.

5 Guwa la nsembe lomwe lamkuwa, adalipanga Bezaleli mwana wa Uri mwana wa Huri linali komweko, ku khomo la kacisi wa Yehova; ndipo Solomo ndi khamulo anafunako.

6 Nakwerako Solomo ku guwa la nsembe pamaso pa Yehova linali ku cihema cokomanako, napereka pamenepo nsembe zopsereza cikwi cimodzi.

7 Usiku womwewo Mulungu anaonekera kwa Solomo, nati kwa iye, Pempha comwe ndikupatse.

8 Nati Solomo kwa Mulungu, Mwacitira Davide atate wanga zokoma zambiri, ndipo mwandiika mfumu m'malo mwace.

9 Tsopano, Yehova Mulungu, likhazikike lonjezano lanu la kwa Davide atate wanga; pakuti mwandiika mfumu ya anthu akucuruka ngati pfumbi lapansi.

10 Mundipatse tsono nzeru ndi cidziwitso, kuti ndituruke ndi kulowa pamaso pa anthu awa; pakuti angathe ndani kuweruza anthu anu awa ambiri?

11 Ndipo Mulungu anati kwa Solomo, Popeza cinali mumtima mwako ici, osapempha cuma, akatundu, kapena ulemu, kapena moyo wa iwo akudana nawe, osapemphanso masiku ambiri; koma wadzipemphera nzeru ndi cidziwitso, kuti uweruze anthu anga amene ndakuika ukhale mfumu yao,

12 nzeru ndi cidziwitso zipatsidwa kwa iwe, ndidzakupatsanso cuma, ndi akatundu, ndi ulemu, zotere zonga sanakhala nazo mafumu akale usanakhale iwe, ndi akudza pambuyo pako sadzakhala nazo zotero.

13 Momwemo Solomo anadza ku Yerusalemu kucokera ku msanje uli ku Gibeoni, ku khomo la cihema cokomanako; ndipo anacita ufumu pa Israyeli.

14 Ndipo Solomo anasonkhanitsa magareta ndi apakavalo, nakhala nao magareta cikwi cimodzi mphambu mazana anai, ndi apakavalo zikwi khumi ndi ziwiri; nawaika m'midzi ya magareta ndi kwa mfumu ku Yerusalemu.

15 Ndipo mfumu inatero kuti siliva ndi golidi zikhale m'Yerusalemu ngati miyala, ndi kuti mikungudza icuruke ngati mikuyu yokhala kucidikha.

16 Ndi akavalo amene Solomo anali nao anafuma ku Aigupto; amalonda a mfumu anawalandira magulu magulu, gulu liri lonse mtengo wace.

17 Ndipo anatenga naturuka nalo gareta ku Aigupto mtengo wace masekeli a siliva mazana asanu ndi limodzi, ndi kavalo mtengo wace zana limodzi mphambu makumi asanu; momwemo anawaturutsira mafumu onse a Ahiti, ndi mafumu a Aramu, ndi dzanja lao.

2

1 Ndipo a Solomo anati alimangire dzina la Yehova nyumba, ndiponso nyumba ya ufumu wace.

2 Nawerenga Solomo amuna zikwi khumi mphambu makumi asanu ndi limodzi osenza mirimo, ndi amuna zikwi makumi asanu ndi atatu otema mitengo m'mapiri, ndi zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi limodzi kuwayang'anira.

3 Ndipo Solomo anatumiza kwa Huramu mfumu ya Turo, ndi kuti, Monga momwe munacitira Davide atate wanga, ndi kumtumizira mikungudza yommangira nyumba yokhalamo, mundicitire ine momwemo.

4 Taonani, nditi ndilimangire dzina la Yehova Mulungu wanga nyumba, kumpatulira iyo, ndi kufukiza pamaso pace zonunkhira za pfungo lokoma, ndiyo ya mkate woonekera wacikhalire, ndi ya nsembe zopsereza, m'mawa ndi madzulo, pamasabata, ndi pokhala mwezi, ndi pa madyerero oikika a Yehova Mulungu wathu. Ndiwo macitidwe osatha m'Israyeli.

5 Ndipo nyumba nditi ndimangeyi ndi yaikuru; pakuti Mulungu wathu ndiye wamkuru woposa milungu yonse.

6 Koma ali nayo mphamvu ndani yakummangira Iye nyumba, popeza thambo lam'mwambamwamba silimfikira? ndine yani ine tsono, kuti ndimmangire nyumba, koma kumfukizira cofukiza ndiko?

7 Ndipo tsono munditumizire munthu wa luso lakucita ndi golidi, ndi siliva, ndi mkuwa, ndi citsulo, ndi thonje lofiirira, ndi lofiira, ndi lamadzi, wakudziwa kuzokota zozokota ziri zonse, akhale ndi amuna aluso okhala ndi ine m'Yuda ndi m'Yerusalemu, amene Davide atate wanga anawakonzeratu.

8 Munditumizirenso mitengo yamikungudza, ndi yamlombwa, ndi yambawa, ya ku Lebano; pakuti ndidziwa kuti anyamata anu adziwa kutema mitengo m'Lebano; ndipo taonani, anyamata anga adzakhala ndi anyamata anu,

9 ndiko kundikonzera mitengo yambirimbiri; pakuti nyumbayi nditi ndiimange idzakhala yaikuru ndi yodabwitsa.

10 Ndipo taonani, ndidzawapatsa anyamata anu otema akulikha mitengo miyeso ya tirigu wopuntha zikwi makumi awiri, ndi miyeso ya barele zikwi makumi awiri, ndi mitsuko yaikuru ya vinyo zikwi makumi awiri, ndi mitsuko yaikufu ya mafuta zikwi makumi awiri.

11 Ndipo Huramu mfumu ya Turo anayankha ndi kulembera, natumiza kalatayo kwa Solomo, ndi kuti, Powakonda anthu ace Yehova anakulongani mfumu yao.

12 Huramu anatinso, Alemekezedwe Yehova Mulungu wa Israyeli, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi, nampatsa mfumu Davide mwana waluso, wodziwa nzeru ndi waluntha, ammangire Yehova nyumba, ndiponso nyumba ya ufumu wace.

13 Ndipo tsono ndatumiza munthu waluso wokhala Ralo, luntha, Huramu Abi,

14 ndiye mwana wa munthu wamkazi wa ana akazi a Dani, ndipo atate wace ndiye munthu wa ku Turo, wodziwa kucita ndi golidi, ndi siliva, ndi mkuwa, ndi citsulo, ndi mwala, ndi mitengo, ndi thonje lofiirira, ndi lamadzi, ndi bafuta la thonje losansitsa ndi lofiira, ndi kuzokota mazokotedwe ali onse, ndi kulingirira copanga ciri conse; kuti ampatse pokhala pamodzi ndi aluso anu, ndi aluso a mbuye wanga Davide atate wanu.

15 Ndipo tsono tirigu ndi barele, mafuta ndi vinyo, mbuye wanga wanenazi, azitumize kwa anyamata ace;

16 ndipo ife tidzatema mitengo ku Lebano monga mwa kusowa kwanu konse; ndipo tidzabwera nayo kwa inu yoyandamitsa paphaka kufikira ku Yopa; ndipo inu mudzakwera nayo ku Yerusalemu.

17 Ndipo Solomo anawerenga alendo Onse okhala m'dziko la Israyeli, monga mwa mawerengedwe aja atate wace Davide adawawerenga nao, nawapeza afikira zikwi zana limodzi mphambu makumi asanu kudza zitatu ndi mazana asanu ndi limodzi.

18 Ndipo anaika zikwi makumi asanu ndi awiri za iwowa asenze mirimo, ndi zikwi makumi asanu ndi atatu ateme m'mapiri, ndi akapitao zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndilimodzi agwiritse anthu nchito.

3

1 Pamenepo Solomo anayamba kumanga nyumba ya Yehova ku Yerusalemu, m'phiri la Moriya, kumene Mulungu anaonekera kwa Davide atate wace, pamalo pamene Davide anakonzeratu pa dwale la Orinani Myebusi.

2 Nayamba kumanga tsiku laciwiri la mwezi waciwiri, caka cacinai ca ufumu wace.

3 Ndipo maziko adawaika Solomo akumangapo nyumba ya Mulungu ndi awa: utali wace, kuyesa mikono monga mwa muyeso wakale, ndiwo mikono makumi asanu ndi limodzi, ndi kupingasa kwace mikono makumi awiri.

4 Ndi likole linali kukhomo kwa nyumba, m'litali mwace monga mwa kupingasa kwa nyumba munali mikono makumi awiri, ndi msinkhu wace zana limodzi mphambu makumr awiri; ndipo analikuta m'katimo ndi golidi woona.

5 M'nyumba yaikuru tsono anacinga ndi mitengo yamlombwa, imene anaikuta ndi golidi wabwino, nalembapo ngati migwalangwa ndi maunyolo.

6 Ndipo anakuta nyumba ndi miyala ya mtengo wace; ndi golidi wace ndiye golidi wa Parivaimu.

7 Anamamatizanso kacisi, mitanda, ziundo, ndi makoma ace, ndi zitseko zace, ndi golidi; nalemba akerubi pamakoma.

8 Ndipo anamanga malo opatulikitsa, m'litali mwace monga mwa kupingasa kwa nyumba mikono makumi awiri, ndi kupingasa kwace mikono makumi awiri; naikuta ndi golidi wabwino wakufikira matalente mazana asanu ndi limodzi.

9 Ndi kulemera kwace kwa misomali ndiko masekeli makumi asanu a golidi. Ndipo anazikuta ndi golidi zipinda zosanjikizana.

10 Ndipo m'malo opatulikitsa anapanga akerubi awiri, anacita osema, nawakuta ndi golidi.

11 Ndi mapiko a akerubi m'litali mwace ndimo mikono makumi awiri; phiko la kerubi mmodzi mikono isanu, lojima khoma la nyumba; ndi phiko linzace mikono isanu, lokhudzana nalo phiko la kerubi wina.

12 Ndi phiko la kerubi wina mikono isanu lojima khoma la nyumba, ndi phiko linzace mikono isanu lolumikizana ndi phiko la kerubi wina.

13 Mapiko a akerubi awa anafunyululika mikono makumi awiri; ndipo anaima ndi mapazi ao, ndi, nkhope zao zinaloza kukhomo.

14 Ndipo anaomba nsaru yocinga ya thonje lamadzi, ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, naomberamo akerubi.

15 Ndipo anapanga ku khomo la nyumba nsanamira ziwiri za mikono makumi atatu mphambu ziwiri; ndi mutu unakhala pamwamba pa iri yonse ndiwo mikono isanu.

16 Napanga maunyolo onga a m'moneneramo, nawamanga pa mitu ya nsanamirazi, napanga makangaza zana limodzi, nawamanga pamaunyolo.

17 Ndipo anaimiritsa nsanamirazo pakhomo pa Kacisi; imodzi ku dzanja lamanja, ndi inzace ku dzanja lamanzere; nalicha dzina la iyi ya ku dzanja lamanja Yakini, ndi dzina la iyi ya ku dzanja lamanzere Boazi.

4

1 Anapanganso guwa la nsembe lamkuwa, m'litali mwace mikono makumi awiri, ndi kupingasa kwace mikono makumi awiri, ndi msinkhu wace mikono khumi.

2 Anayenganso thawale losungunula la mikono khumi kukamwa, lozunguniza, ndi msinkhu wace mikono isanu; ndi cingweca mikono makumi atatu cinalizunguniza.

3 Ndi pansi pace panali mafanziro a ng'ombe zakulizinga khumi ku mkono umodzi, zakuzinga thawalelo pozungulira pace. Ng'ombezo zinali m'mizere iwiri, zinayengeka poyengedwa thawalelo.

4 Linasanjikika pa ng'ombe khumi ndi ziwiri, zitatu zinapenya kumpoto, ndi zitatu zinapenya kumadzulo, ndi zitatu zinapenya kumwela, ndi zitatu zinapenya kum'mawa; ndi thawale linasanjikika pamwamba pao, ndi nkholo zao zinayang'anana.

5 Ndi kucindikira kwace kunanga cikhato, ndi mlomo wace unasadamuka ngati mlomo wa comwera, ngati luwa la kakombo; analowamo madzi a mitsuko yaikuru zikwi zitatu.

6 Anapanganso mbiya zamphwamphwa khumi, naika zisanu ku dzanja lamanja, ndi zisanu ku dzanja lamanzere, kutsukiramo; za nsembe yopsereza anazitsuka m'menemo; koma thawale ndi la ansembe kusambiramo.

7 Ndipo anapanga zoikapo nyali khumi zagolidi, monga mwa ciweruzo cace; naziika m'Kacisi, zisanu ku dzanja lamanja, ndi zisanu ku dzanja lamanzere.

8 Anapanganso magome khumi, nawaika m'Kacisi, asanu ku dzanja lamanja, ndi asanu ku dzanja lamanzere. Napanga mbale zowazira zana limodzi zagolidi.

9 Anamanganso bwalo la ansembe, ndi bwalo lalikuru, ndi zitseko za kubwalo, nakuta zitseko zace ndi mkuwa.

10 Ndipo anaika thawalelo ku dzanja lamanja la nyumba kum'mawa cakumwela.

11 Ndipo Huramu anapanga miphika, ndi zoolera zace, ndi mbale zowazira zace. Natsiriza Huramu nchito adaicitira mfumu Solomo m'nyumba ya Mulungu:

12 nsanamira ziwiri, ndi zikhozo, ndi mitu iwiri inali pamwamba pa nsanamirazo, ndi maukonde awiri akukuta zikho ziwiri za mitu iri pamwamba pa nsanamirazo,

13 ndi makangaza mazana anai a maukonde awiri wa; mizere iwiri ya makangaza ya ukonde uli wonse, akukuta zikho ziwiri za mitu, inali pa nsanamirazo.

14 Anapanganso maphaka, napanga mbiya zamphwamphwa khumi pamwamba pa maphaka;

15 thawale limodzi ndi ng'ombe khumi ndi ziwiri pansi pace.

16 Miphika yomwe, ndi zoolera, ndi mitungo, ndi zipangizo zace zonse, Huramu Abi anazipangira mfumu Solomo, kuzipangira nyumba ya Yehova, za mkuwa wonyezimira.

17 Mfumuyi inaziyenga pa cidikha ca ku Yordano, m'dothi ladongo, pakati pa Sukoti ndi Zereda.

18 Ndipo Solomo anazipanga zipangizo izi zonse zocurukadi, pakuti kulemera kwace kwa mkuwa sikunayeseka.

19 Solomo anapanganso zipangizo zonse zinali m'nyumba ya Mulungu, guwa la nsembe lagolidi lomwe, ndi magome oikapo mkate woonekera;

20 ndi zoikapo nyali ndi nyali zace za golidi woona, zakuunikira monga mwa cilangizo cace cakuno ca moneneramo;

21 ndi maluwa, ndi nyali, ndi mbano zagolidi, ndiwo golidi wangwiro;

22 ndi zozimira nyali, ndi mbale zowazira, ndi zipande, ndi mbale za zofukiza za golidi woona; ndi kunena za polowera m'nyumba, zitseko zace za m'katimo za malo opatulikitsa, ndi zitseko za nyumbayi, ndiyo Kacisi, zinali zagolidi.

5

1 Momwemo zidatha nchito zonse Solomo adazicitira nyumba ya Yehova. Ndipo Solomo anabwera nazo zopatulika zija za atate wace Davide; naziika siliva, ndi golidi, ndi zipangizo zonse m'cuma ca nyumba ya Mulungu. Kuperekedwa kwa Kacisi.

2 Pamenepo Solomo anasonkhanitsira akulu akulu a Israyeli, ndi akuru onse a mafuko, ndi akalonga a nyumba za makolo a ana a Israyeli, ku Yerusalemu, kukatenga likasa la cipangano ca Yehova ku mudzi wa Davide ndiwo Zioni.

3 Ndipo amuna onse a Israyeli anasonkhana kwa mfumu kumadyerero anacitikawo, m'mwezi wacisanu ndi ciwiri.

4 Nadza akulu akulu onse a Israyeli, nanyamula likasalo Alevi.

5 Ndipo anakwera nalo likasa, ndi cihema cokomanako, ndi zipangizo zonse zopatulika zinali m'cihemamo; izizo ansembe Alevi anakwera nazo.

6 Ndi mfumu Solomo ndi khamu lonse la Israyeli losonkhana kwa iye anali kulikasa, naphera nsembe, nkhosa ndi ng'ombe zosawerengeka kucuruka kwace.

7 Ndipo ansembe analowa nalo likasa la cipangano la Yehova kumalo kwace m'moneneramo mwa kacisi, m'malo opatulikitsa, pansi pa mapiko a akerubi.

8 Pakuti akerubi anafunyulula mapiko ao pa malo a likasa, ndi akerubi anaphimba likasa ndi mphiko zace pamwamba pace.

9 Ndipo zinatalikitsa mphikozo, kuti nsonga za mphiko zidaoneka kulikasa cakuno ca moneneramo, koma sizinaoneka kubwalo; ndipo ziri komweko mpaka lero lino.

10 Munalibe kanthu kena m'likasa, koma magome awiri Mose anawaika m'mwemo ku Horebu, muja Yehova anacita cipangano ndi ana a Israyeli poturuka iwo m'Aigupto.

11 Ndipo ansembe anaturuka m'malo opatulika, pakuti ansembe onse anali komwe adadzipatula, osasunga magawidwe ao;

12 Alevi omwe akuyimba, onsewo ndiwo Asafu, Hemani, Yedutuni, ndi ana ao, ndi abale ao obvala bafuta, ali nazo nsanje, ndi zisakasa, ndi azeze, anaima kum'mawa kwa guwa la nsembe, ndi pamodzi nao ansembe zana limodzi mphambu makumi awiri akuomba malipenga.

13 Ndipo kunali, pakucita limodzi amalipenga ndi oyimba, kumveketsa mau amodzi akulemekeza ndi kuyamika Yehova, ndi pakukweza mau ao pamodzi ndi malipenga, ndi nsanje, ndi zoyimbira zina, ndi kulemekeza Yehova, ndi kuti, Pakuti Iye ndiye wabwino, pakuti cifundo cace cikhala cikhalire; pamenepo mtambo unadzaza nyumbayi, ndiyo nyumba ya Yehova;

14 ndipo ansembe sanakhoza kuimirira kutumikira cifukwa ca mtambowo; pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza nyumba ya Mulungu.

6

1 Pamenepo Solomo anati, Yehova anati kuti adzakhala mu mdima wandiweyani.

2 Koma ndakumangirani nyumba yokhalamo, malo okhazikika okhalamo Inu nthawi yosatha.

3 Ndipo mfumu inapotolokera nkhope yace, nidalitsa khamu lonse la Israyeli; ndi khamu lonse la Israyeli linaimirira.

4 Nati iye, Alemekezedwe Yehova Mulungu wa Israyeli, wakunena m'kamwa mwace ndi Davide atate wanga, nakwaniritsa: ndi manja ace, ndi kuti,

5 Kuyambira tsiku lakuturutsa Ine anthu anga m'dziko la Aigupto, sindinasankha mudzi uli wonse m'mafuko onse a Israyeli, kumangamo nyumba yokhalamo dzina langa, kapena kusankha munthu ali yense akhale kalonga wa anthu anga Israyeli;

6 koma ndinasankha Yerusalemu, kuti dzina langa likhale komweko; ndinasankhanso Davide akhale mfumu ya anthu anga Israyeli.

7 Ndipo Davide atate wanga anafuna mumtima mwace kumangira dzina la Yehova Mulungu wa Israyeli nyumba.

8 Koma Yehova anati kwa Davide atate wanga, Popeza unafuna mumtima mwako kulimangira dzina langa nyumba, unacita bwino kuti unatero mumtima mwako;

9 koma sudzandimangira nyumba ndiwe, koma mwana wako wakudzaturuka m'cuuno mwako, Iyeyo adzalimangira dzina langa nyumbayi.

10 Ndipo Yehova wakhazikitsa mau ace adanenawo, pakuti ndinauka ine m'malo mwa Davide atate wanga, ndipo ndikhala pa mpando wacifumu wa Israyeli monga analonjeza Yehova, ndipo ndamangira dzina la Yehova Mulungu wa Israyeli nyumbayi.

11 Ndipo ndalongamo likasa, muli cipangano ca Yehova, anacicita ndi ana a Israyeli.

12 Ndipo Solomo anaima ku guwa la nsembe la Yehova pamaso pa khamu lonse la Israyeli, natambasula manja ace.

13 Ndipo Solomo adapanga ciunda camkuwa, m'litali mwace mikono isanu, ndi kupingasa kwace mikono isanu, ndi msinkhu wace mikono itatu, naciika pakati pa bwalo; ndipo anaima pamenepo, nagwada pa maondo ace pamaso pa khamu lonse la Israyeli, natambasulira manja ace kumwamba;

14 nati, Yehova. Mulungu wa Israyeli, palibe Mulungu ngati Inu, m'mwamba, kapena pa dziko lapansi, wakusungira cipangano ndi cifundo akapolo anu akuyenda pamaso panu ndi mtima wao wonse;

15 inu amene mwasungira mtumiki wanu Davide atate wanga cija mudamlonjezaci: inde munanena ndi pakamwa panu, ndipo mwacita ndi dzanja lanu, monga momwe muli lero lino.

16 Ndipo tsopano, Yehova Mulungu wa Israyeli, msungireni mtumiki wanu Davide cija mudamlonjezaco, ndi kuti, Sadzakusowa munthu pamaso panga wakukhala pa mpando wacifumu wa Israyeli; pokhapo ngati ana ako asamalira njira yao, kuti ayende m'cilamulo canga, monga umo unayendera iwe pamaso panga.

17 Ndipo tsopano, Yehova Mulungu wa Israyeli, acitike mau anu amene munanena kwa Davide mtumiki wanu.

18 Koma kodi nzoona kuti Mulungu akhala ndi anthu pa dziko lapansi? taonani, thambo, inde m'mwambamwamba, sizifikira inu, koposa kotani nanga nyumba iyi ndaimanga?

19 Cinkana citero, labadirani pemphero la kapolo wanu, ndi pembedzero lace, Yehova Mulungu wanga, kumvera kupfuula ndi kupempha kwace, kumene kapolo wanu apempha pamaso panu;

20 kuti maso anu atsegukire nyumba iyi usana ndi usiku, malo amene munanenerako kuti mudzaikako dzina lanu, kuti mumvere pemphero limene kapolo wanu adzapempha kuloza konkuno.

21 Ndipo mverani mapembedzero a kapolo wanu ndi a anthu anu Israyeli, popemphera iwo kuloza konkuno; ndipo mumvere Inu m'Mwamba mokhala Inumo, ndipo pakumva Inu, mukhululikire.

22 Munthu akacimwira mnansi wace, ndipo akamuikira lumbiro lakumlumbiritsa, ndipo akadzalumbira ku guwa lanu la nsembe, m'nyumba yino;

23 pamenepo mumvere m'Mwamba, nimucite ndi kuweruzira akapolo anu, kumtsutsa woipayo, ndi kumbwezera chimo lace, ndi kulungamitsa wolungamayo, kumbwezera monga mwa cilungamo cace.

24 Ndipo anthu anu Israyeli akawakantha mdani cifukwa ca kukucimwirani, nakabwerera iwowa ndi kubvomereza dzina lanu, ndi kupemphera, ndi kupembedzera pamaso panu m'nyumba yino;

25 pamenepo mumvere Inu m'Mwamba, nimukhululukire chimo la anthu anu Israyeli, ndi kuwabwezera ku dziko limene munapatsa makolo ao.

26 Mukatsekeka m'mwamba, mopanda mvula, cifukwa ca kukucimwirani; akapemphera iwo kuloza kumalo kuno, ndi kubvomereza dzina lanu, ndi kutembenuka kwa zoipa zao, pamene muwasautsa;

27 pamenepo mumvere Inu m'Mwamba, nimukhululukire chimo la akapolo anu, ndi la anthu anu Israyeli, mutawalangiza njira, yokoma ayenera kuyendamo, nimutumizire mvula dziko lanu limene munapatsa anthu anu likhale colowa cao.

28 Mukakhala njala m'dzikomo, mukakhala mliri, mukakhala cinsikwi, kapena cinoni, dzombe, kapena kapuce; akawamangira misasa adani ao, m'dziko la midzi yao; mukakhala mliri uli wonse, kapena nthenda iri yonse;

29 pemphero ndi pembedzero liri lonse likacitika ndi munthu ali yense, kapena ndi anthu anu onse Aisrayeli, akadziwa yense cinthenda cace, ndi cisoni cace, nakatambasulira manja ace kuloza ku nyumba iyi;

30 pamenepo mumvere m'Mwamba mokhala Inumo, nimukhululukire, ndi kubwezera ali yense monga mwa njira zace zonse, monga mudziwa mtima wace; pakuti Inu, Inu nokha, mudziwa mitima ya ana a anthu;

31 kuti aope Inu, kuyenda m'njira zanu masiku onse akukhala iwo m'dziko limene munapatsa makolo athu.

32 Ndiponso kunena za mlendo wosakhala wa anthu anu Israyeli, akafumira ku dziko lakutari cifukwa ca dzina lanu lalikuru, ndi dzanja lanu lamphamvu, ndi mkono wanu wotambasuka; akadza iwowa ndi kupemphera kuloza ku nyumba iyi;

33 pamenepo mumvere Inu m'Mwamba mokhala Inumo, nimumcitire mlendoyo monga mwa zonse akuitanirani; kuti mitundu yonse ya anthu a pa dziko lapansi adziwe dzina lanu, nakuopeni, monga amatero anthu anu Aisrayeli; ndi kuti adziwe kuti nyumba iyi ndamangayi ichedwa ndi dzina lanu.

34 Akaturukira kunkhondo anthu anu kuyambana ndi adani ao, kutsata njira iri yonse muwatumiza; nakapemphera kwa Inu kuloza ku mudzi uwu munausankha, ndi nyumba iyi ndaimangira dzina lanu;

35 pamenepo mumvere m'Mwamba pemphero lao ndi pembedzero lao, ndi kulimbitsa mlandu wao.

36 Akacimwira Inu (pakuti palibe munthu wosacimwa), nimukakwiya nao, ndi kuwapereka kwa adani, kuti awatenge andende kumka nao ku dziko lakutali, kapena lapafupi;

37 koma akalingirira m'mtima mwao kudziko kumene anawatengera andende, nakatembenuka, nakapembedzera Inu m'dziko la undende wao, ndi kuti, Tacimwa, tacita mphulupulu, tacita coipa;

38 akabwerera kwa Inu ndi mtima wao wonse, ndi moyo wao wonse, m'dziko la undende wao, kumene adawatengera andende; nakapemphera kuloza ku dziko lao limene munapatsa makolo ao, ndi mudzi mudausankha, ndi kunyumba ndamangira dzina lanuyi;

39 pamenepo mumvere Inu m'Mwamba mokhala Inumo pemphero lao ndi pembedzero lao, ndi kulimbitsa mlandu wao; nimukhululukire anthu anu amene anakucimwirani.

40 Tsopano Mulungu wanga, maso anu akhale cipenyere, ndi makutu anu cimvere, pemphero locitika pamalo pano.

41 Ndipo tsopano nyamukani, Yehova Mulungu, kudza kopumulira kwanu, Inu ndi likasa la mphamvu yanu; ansembe anu, Yehova Mulungu, abvale cipulumutso; ndi okondedwa anu akondwere nazo zabwino.

42 Yehova Mulungu, musabweza nkhope ya wodzozedwa wanu, mukumbukile zacifundo za Davide mtumiki wanu.

7

1 Atatha tsono Solomo kupemphera, moto unatsika kumwamba, nunyeketsa nsembe yopsereza, ndi nsembe zophera; ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza nyumbayi.

2 Ndipo ansembe sanakhoza kulowa m'nyumba ya Yehova, popeza ulemerero wa Yehova unadzaza nyumba ya Yehova.

3 Ndi ana onse a Israyeli anapenyerera potsika motowo, ndi pokhala ulemerero wa Yehova panyumbayi; nawerama nkhope zao pansi poyalidwa miyala, nalambira, nayamika Yehova, nati, Pakuti Iye ndiye wabwino, pakuti cifundo cace cikhala cikhalire.

4 Pamenepo mfumu ndi anthu onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova.

5 Ndipo mfumu Solomo anapereka nsembe ya ng'ombe zikwi makumi awiri mphambu ziwiri, ndi nkhosa zikwi, makumi awiri. Momwemo mfumu ndi anthu onse anapereka nyumba ya Yehova.

6 Naimirira ansembe m'udikiro wao; ndi Alevi omwe ndi zoyimbira za Yehova, adazipanga Davide mfumu kuyamika nazo Yehova, pakuti cifundo cace cikhala cikhalire, polemekeza Davide mwa utumiki wao; ndi ansembe anaomba malipenga pamaso pao, nakhala ciriri Israyeli yense.

7 Ndipo Solomo anapatula pakati pace pa bwalo liri pakhomo pa nyumba ya Yehova; pakuti anapereka nsembe zopsereza, ndi mafuta a nsembe zoyamika pomwepo; popeza guwa la nsembe lamkuwa adalipanga Solomo linacepa kulandira nsembe yopsereza, ndi nsembe yaufa, ndi mafuta.

8 Nthawi yomweyo Solomo anacita madyerero masiku asanu ndi awiri, ndi Aisrayeli onse pamodzi naye, khamu lalikuru ndithu, kuyambira polowera ku Hamati kufikira mtsinje wa ku Aigupto.

9 Ndipo tsiku lacisanu ndi citatu anacita msonkhano woletsa; popeza anacita zakupereka guwa la nsembe masiku asanu ndi awiri, ndi madyerero masiku asanu ndi awiri.

10 Ndipo tsiku la makumi awiri ndi citatu la mwezi wacisanu ndi ciwiri anawauza anthu apite ku mahema ao, akusekera ndi kukondwera m'mtima mwao cifukwa ca zokoma Yehova adawacitira Davide, ndi Solomo, ndi Aisrayeli anthu ace.

11 Momwemo Solomo anatsiriza nyumba ya Yehova, ndi nyumba ya mfumu; ndipo ziri zonse zidalowa mumtima mwace mwa Solomo kuzicita m'nyumba ya Yehova, ndi m'nyumba yace yace, anacita mosabwezeza.

12 Ndipo Yehova anaonekera kwa Solomo usiku, nanena naye, Ndamva pemphero lako, ndadzisankhira malo ano akhale nyumba ya nsembe.

13 Ndikatseka kumwamba kuti pasakhale mvula, kapena ndikalamulira dzombe lithe za padziko, kapena ndikatumiza mliri mwa anthu anga;

14 ndipo anthu anga ochedwa dzina langa akadzicepetsa, nakapemphera, nakafuna nkhope yanga, nakatembenuka kuleka njira zao zoipa; pamenepo ndidzamvera m'Mwamba, ndi kukhululukira coipa cao, ndi kuciritsa dziko lao.

15 Tsopano maso anga adzakhala otsegukira, ndi makutu anga ochera, pemphero la m'malo ano.

16 Pakuti ndasankha ndi kuipatula nyumba Iyi, kuti dzina langa likhaleko cikhalire; inde maso anga ndi mtima wanga zidzakhala komweko kosalekeza.

17 Ndipo iwe ukadzayenda pamaso panga monga umo anayendera Davide atate wako, nukacita monga mwa zonse ndakulamulira iwe, nukasunga malemba anga ndi maweruzo anga;

18 pamenepo ndidzakhazikitsa mpando wacifumu wa ufumu wako, monga ndinapangana ndi Davide atate wako, ndi kuti, Sadzakusowa munthu wokhala mfumu m'Israyeli.

19 Koma mukabwerera inu, ndi kusiya malemba anga, ndi malamulo anga, amene ndaika pamaso panu, ndi kumuka ndi kutumikira milungu yina ndi kuilambira;

20 pamenepo ndidzawazula m'dziko langa limene ndinawapatsa; ndi nyumba yino ndinaipatulira dzina langa ndidzaitaya, osaionanso, ndi kuiyesa mwambi ndi mnyozo mwa mitundu yonse ya anthu.

21 Ndi munthu yense wakupita pa nyumba iyi yaitali adzadabwa nayo, nadzati, Yeliova ana tero ndi dziko lino ndi nyumba yino cifukwa ninji?

22 Ndipo adzayankha, Popeza anasiya Yehova Mulungu wa makolo ao amene anawaturutsa m'dziko la Aigupto, nagwira milungu yina, nailambira ndi kuitumikira; cifukwa cace anawagwetsera coipa ici conse.

8

1 Ndipo kunali, zitatha zaka makumi awiri m'mene anamanga nyumba ya Yehova, ndi nyumba yace yace,

2 Solomo anamanga midzi imene Huramu adampatsa, nakhalitsamo ana a Israyeli.

3 Ndipo Solomo anamuka ku Hamati Zoba, naugonjetsa.

4 Ndipo anamanga Tadimori m'cipululu, ndi midzi yonse yosungiramo cuma, imene anaimanga m'Hamati.

5 Anamanganso Betihoroni wa kumtunda, ndi Betihoroni wa kunsi, midzi ya malinga yokhala nao malinga, zitseko, ndi mipiringidzo;

6 ndi Balati, ndi midzi yonse yosungiramo cuma anali nayo Solomo, ndi midzi yonse ya magareta ace, ndi midzi ya apakavalo ace, ndi zonse anazifuna Solomo kuzimanga zomkondweretsa m'Yerusalemu, ndi m'Lebano, ndi m'dziko lonse la ufumu wace.

7 Ndipo anthu onse otsala mwa Ahiti, ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi, osati Aisrayeli,

8 mwa ana ao otsala m'dziko pambuyo pao, amene ana a Israyeli sanawatha, mwa iwowa Solomo anawacititsa thangata mpaka lero lino.

9 Koma mwa ana a Israyeli Solomo sanawayesa akapolo omgwirira nchito; koma iwowa anali anthu a nkhondo, akazembe ace akuru, ndi akuru a magareta ace, ndi apakavalo ace.

10 Amenewa anali akuru a akapitao a mfumu Solomo, ndiwo mazana awiri mphambu makumi asanu akulamulira anthu.

11 Ndipo Solomo anamkweretsa mwana wamkazi wa Farao m'mudzi wa Davide, alowe m'nyumba imene adammangira; pakuti anati, Mkazi wanga asakhale m'nyumba ya Davide mfumu ya Israyeli; popeza mpopatulika pamene panafika likasa la Yehova.

12 Pamenepo Solomo anapereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa la nsembe la Yehova, limene adalimanga pakhomo palikole,

13 monga momwe mudayenera, tsiku ndi tsiku; napereka monga momwe adauza Mose pamasabata, pokhala mwezi, ndi pa madyerero oikika, katatu m'caka, pa madyerero ali mkate wopanda cotupitsa, ndi pa madyerero a masabata, ndi pa madyerero a misasa.

14 Ndipo anaika monga mwa ciweruzo ca Davide atate wace zigawo za ansembe ku utumiki wao, ndi Alevi ku udikiro wao, kulemekeza Mulungu, ndi kutumikira pamaso pa ansembe, monga munayenera tsiku ndi tsiku; odikira omwe monga mwa zigawo zao ku cipata ciri conse; pakuti momwemo Davide munthu wa Mulungu adamuuza.

15 Ndipo sanapambuka pa lamulo la mfumu la kwa ansembe ndi Alevi, kunena za kanthu kali konse, kapena za cumaci.

16 Momwemo nchito yonse ya Solomo inakonzekeratu tsiku lakuika maziko a nyumba ya Yehova, mpaka anaitsiriza.

17 Pamenepo Solomo anamuka ku Ezioni Geberi, ndi ku Eloti pambali pa nyanja, m'dziko la Edomu.

18 Ndipo Huramu anamtumizira zombo, ndi amarinyero ace, ndi anyamata akudziwa za m'nyanja; ndipo anamuka pamodzi ndi anyamata a Solomo ku Ofiri, natengako matalente mazana anai mphambu makumi asanu a golidi, nabwera nao kwa Solomo mfumu.

9

1 Ndipo atamva mfumu yaikazi ya ku Seba mbiri ya Solomo, anadza kumuyesera Solomo ndi miyambi yododometsa ku Yerusalemu, ndi ulendo waukuru, ndi ngamila zosenza zonunkhira, ndi golidi wocuruka, ndi timiyala ta mtengo wace; ndipo atafika kwa Solomo anakamba naye zonse za m'mtima mwace.

2 Ndipo Solomo anammasulira mau ace onse, panalibe kanthu kombisikira Solomo, kamene sanammasulira.

3 Ndipo mfumu yaikazi ya ku Seba ataiona nzeru ya Solomo, ndi nyumba adaimanga,

4 ndi zakudya za pa gome lace, ndi makhalidwe a anyamata ace, ndi maimiriridwe a atumiki ace, ndi mabvalidwe ao, ndi otenga zikho ace, ndi mabvalidwe ao, ndi makweredwe ace pokwera iye kumka ku nyumba ya Yehova, munalibenso moyo mwa iye.

5 Ndipo anati kwa mfumu, Inali yoona mbiri ija ndidaimva m'dziko langa, ya macitidwe anu, ndi ya nzeru zanu.

6 Koma sindinakhulupira mau ao mpaka ndinadza, ndaona ndi maso anga; ndipo taonani anandifotokozera dera lina lokha la nzeru zanu zocuruka; mwa, onjezatu pa mbiri ndidaimva.

7 Odala anthu anu, ndi odala anyamata anu awa akuima ciimirire pamaso panu, ndi kumva nzeru zanu.

8 Wolemekezeka Yehova Mulungu wanu, wakukondwera nanu, kukuikani pa mpando wacifumu wace, mukhalire Yehova Mulungu wanu mfumu pa anthu ace; popeza Mulungu wanu anakonda Aisrayeli kuwakhazika kosatha, anakulongani mfumu yao, kucita ciweruzo ndi cilungamo.

9 Ndipo mkaziyo anapatsa mfumu matalente a golidi zana limodzi mphambu makumi awiri, ndi zonunkhira zambiri ndithu, ndi timiyala ta mtengo wace; panalibe zonunkhira zina zonga zija mfumu yaikazi ya ku Seba anapatsa mfumu Solomo.

10 Ndiponso anyamata a Huramu, ndi anyamata a Solomo otenga golidi ku Ofiri, anatenga mitengo yambawa ndi timiyala ta mtengo wapatali.

11 Ndipo mfumu inasema mitengo yambawa ikhale mizati ya nyumba ya Yehova, ndi nyumba ya mfumu, ndi azeze, ndi zisakasa za oyimbira; sizinaoneka zotere ndi kale lonse m'dziko la Yuda.

12 Ndipo mfumu Solomo anampatsa mfumu yaikazi ya ku Seba cifuniro cace conse, ciri conse anacipempha, osawerengera zija adabwera nazo kwa mfumu. Momwemo anabwerera, namuka ku dziko lace, iyeyu ndi anyamata ace.

13 Kulemera kwace tsono kwa golidi anafika kwa Solomo caka cimodzi ndiko matalente mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi limodzi a golidi;

14 osawerenga uja anabwera naye amalonda oyendayenda, ndi amalonda ena; ndipo mafumu onse a Arabiya, ndi akazembe a dziko, anadza naye golidi ndi siliva kwa Solomo.

15 Ndipo mfumu Solomo anapanga zikopa mazana awiri za golidi wonsansantha, cikopa cimodzi cinathera golidi wonsansantha masekeli mazana awiri.

16 Napanganso malihawo mazana atatu a golidi wonsansantha, cikopa cimodzi cinathera masekeli mazana atatu a golidi; ndipo mfumu inazilonga m'nyumba yochedwa Nkhalango ya Lebano.

17 Mfumu inapanganso mpando wacifumu waukuru wa minyanga, naukuta ndi golidi woona.

18 Ndi mpando wacifumuwo unali nao makwerero asanu ndi limodzi, ndi copondapo mapazi cagolidi, omangika ku mpandowo; ndi ku mbali zonse ziwiri za pokhalirapo kunali manja; ndi mikango iwiri inaimirira m'mbali mwa manjawo.

19 Ndi mikango khumi ndi iwiri Inaimirirapo, mbali yina ndi yina, pa makwerero asanu ndi limodzi; sanapangidwa wotere m'ufumu uli wonse.

20 Ndipo zikho zomwera zonse za Solomo zinali zagolidi, ndi zipangizo zonse za nyumba yochedwa Nkhalango ya Lebano zinali za golidi woona; siliva sanayesedwa kanthu m'masiku a Solomo.

21 Pakuti zombo za mfumu zinayenda ku Tarisi ndi anyamata a Huramu; zombo za ku Tarisi zinadza kamodzi zitapita zaka zitatu, ndi kubwera nazo golidi, ndi siliva, minyanga, ndi apusi, ndi mbalame za zitsukwa zazitali za mawanga mawanga.

22 Mamwemo mfumu Solomo inaposa mafumu onse a pa dziko lapansi, kunena za cuma ndi nzeru.

23 Ndipo mafumu onse a pa dziko lapansi anafuna nkhope ya Solomo, kudzamva nzeru zace Mulungu adazilonga m'mtima mwace.

24 Nabwera nao munthu yense mtulo wace, zipangizo zasiliva, ndi zipangizo zagolidi, zobvala, ndi zobvala za nkhondo, ndi zonunkhira, akavalo, ndi nyuru; momwemo caka ndi caka.

25 Ndipo Solomo anali nazo zipinda zikwi zinai za akavalo ndi magareta, ndi apakavalo zikwi khumi ndi ziwiri; nawaika m'toidzi ya magareta, ndi m'Yerusalemu kwa mfumu.

26 Ndipo analamulira mafumu onse kuyambira ku Firate kufikira ku dziko la Afilisti, ndi ku malire a ku Aigupto.

27 Ndipo mfumu inacurukitsa siliva m'Yerusalemu ngati miyala; ndi mikungudza anailinganiza ndi mikuyu iri kumadambo kucuruka kwace.

28 Ndipo anakamtengera Solomo akavalo ku Aigupto, ndi ku maiko onse.

29 Macitidwe ena tsono a Solomo, oyamba ndi otsiriza, salembedwa kodi m'buku la mau a Natani mneneri ndi m'zonenera za Ahiya wa ku Silo, ndi m'masomphenya a Ido mlauli za Yerobiamu mwana wa Nebati?

30 Ndipo Solomo anakhala mfumu ya Israyeli yense m'Yerusalemu zaka makumi anai.

31 Nagona Solomo pamodzi ndi makolo ace, naikidwa m'mudzi wa Davide atate wace; ndipo Rehabiamu mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

10

1 Ndipo Rehabiamu anamuka ku Sekemu; pakuti Aisrayeli onse adadza ku Sekemu kumlonga ufumu.

2 Ndipo kunali, atamva Yerobiamu mwana wa Nebati (popeza anali m'Aigupto kumene adathawira, kuthawa Solomo mfumu), Yerobiamu anabwera kucoka ku Aigupto.

3 Ndipo anatuma munthu kukamuitana, nadza Yerobiamu ndi Aisrayeli onse, nalankhula ndi Rehabiamu, ndi kuti,

4 Atate wanu analemeretsa goli lathu; inu tsono pepuzaniko nchito yolemetsa ya atate wanu, ndi goli lace lolemera anatisenzetsali, ndipo tidzakutumikirani.

5 Ndipo ananena nao, Mubwerenso atapita masiku atatu. Nacoka anthu.

6 Ndipo Rehabiamu mfumu anafunsana ndi akulu akulu, amene anaimirira pamaso pa Solomo atate wace akali ndi moyo, nati, Mundipangire bwanji, kuti ndiwabwezere mau anthu awa?

7 Ndipo ananena naye, kuti, Mukawacitira cokoma anthu awa, ndi kuwakonda, ndi kulankhula nao mau okoma, adzakhala anyamata anu kosatha.

8 Koma analeka uphungu wa akulu akuluwa adampangirawo, nakafunsana ndi anyamata anakula naye pamodzi, oimirira pamaso pace.

9 Nati nao, Mundipangire bwanji inu, kuti tibwezere mau anthu awa ananena nanewo, ndi kuti, Mupepuze goli limene atate wanu anatisenzetsa ife?

10 Ndipo anyamatawo adakula naye pamodzi ananena naye, ndi kuti, Muzitero nao anthu awa adalankhula nanu, ndi kuti, Atate wanu analemeretsa goli lathu, koma inu mutipepuzire ilo; muzitero nao, Kanense wanga adzaposa m'cuuno mwa atate wanga.

11 Ndipo tsopano, popeza atate wanga anakusenzetsani goli lolemera, ine ndidzaonjezerapo pa goli lanu; atate wanga anakukwapulani ndi zikoti, koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.

12 Tsono Yerobiamu ndi anthu onse anabwera kwa Rehabiamu tsiku lacitatu, monga mfumu idanena, ndi kuti, Bweraninso kwa ine tsiku lacitatu.

13 Ndipo mfumu inawayankha mokaripa, popeza mfumu Rehabiamu analeka uphungu wa akulu akulu,

14 nalankhula nao monga umo anampangira acinyamata, ndi kuti, Atate wanga analemeretsa goli lanu, koma ine ndidzaonjezerapo; atate wanga anakukwapulani ndi zikoti, koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.

15 Momwemo mfumu siinamvera anthuwo; pakuti kusinthaku kudafuma kwa Mulungu, kuti Yehova akhazikitse mau ace, amene ananenetsa Ahiya wa ku Silo kwa Yerobiamu mwana wa Nebati.

16 Ndipo pakuona Aisrayeli onse kuti mfumu sinawamvera anthuwo, anamyankha mfumu, ndi kuti, Tiri naye ciani Davide? inde tiribe colowa m'mwana wa Jese; tiyeni kwathu, Aisrayeli inu; yang'anira nyumba yako tsopano, Davide. Momwemo Aisrayeli onse anamuka ku mahema ao.

17 Koma za ana a Israyeli okhala m'midzi ya Yuda, Rehabiamu anakhalabe mfumu yao.

18 Pamenepo Rehabiamu mfumu inatuma Hadoramu woyang'anira thangata; koma ana a Israyeli anamponya miyala, nafa. Ndipo Rehabiamu mfumu anafulumira kukwera pa gareta wace kuthawira ku Yerusalemu.

19 Motero Israyeli anapandukana nayo nyumba ya Yuda mpaka lero lino.

11

1 Ndipo atafika ku Yerusalemu Rehabiamu, anamemeza a nyumba ya Yuda ndi Benjamini amuna osankhika zikwi zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu, ndiwo ankhondo, alimbane ndi Aisrayeli kubwezanso ufumu kwa Rehabiamu.

2 Koma mau a Yehova anadza kwa Semaya munthu wa Mulunguyo, ndi kuti,

3 Lankhula ndi Rehabiamu mwana wa Solomo mfumu ya Yuda ndi Benjamini, ndi kuti,

4 Atero Yehova, Musamuka kukayambana ndi abale anu, bwererani yense ku nyumba yace; pakuti cinthu ici cifuma kwa Ine. Ndipo anamvera mau a Yehova, nabwerera osakayambana ndi Yerobiamu.

5 Ndipo Rehabiamu anakhala m'Yerusalemu, namanga midzi yolimbikiramo m'Yuda.

6 Anamangadi Betelehemu, ndi Etamu, ndi Tekoa,

7 ndi Betezuri, ndi Soko, ndi Adulamu,

8 ndi Gati, ndi Maresa, ndi Zifi,

9 ndi Adoraimu, ndi Lakisi, ndi Azeka,

10 ndi Zora, ndi Ayaloni, ndi Hebroni; ndiyo midzi yamalinga ya m'Yuda ndi Benjamini.

11 Ndipo analimbitsa malingawo, naikamo atsogoleri, ndi cakudya cosungikiratu, ndi mafuta, ndi lvinyo.

12 Ndi m'midzi iri yonse anaikamo zikopa ndi mikondo, nailimbitsa cilimbitsire. Ndipo Yuda ndi Benjamini anakhala ace.

13 Ndipo ansembe ndi Alevi okhala m'Israyeli lonse anadziphatikiza kwa iye, ocokera m'malire ao Onse.

14 Pakuti Alevi anasiya podyetsa pao, ndi maiko ao ao, nadza ku Yuda ndi ku Yerusalemu; popeza Yerobiamu ndi ana ace anawataya, kuti asacitire Yehova nchito ya nsembe;

15 nadziikira ansembe a misanje, ndi a ziwanda, ndi a ana a ng'ombe adawapanga.

16 Ndipo akuwatsata iwo anadza ku Yerusalemu, ocokera m'mafuko onse a Israyeli, iwo akupereka mitima yao kufuna Yehova Mulungu wa Israyeli, kudzaphera Yehova Mulungu wa makolo ao nsembe.

17 Momwemo analimbikitsa ufumu wa Yuda, nalimbikitsa Rehabiamu, mwana wa Solomo zaka zitatu; pakuti anayenda m'njira ya Davide ndi Solomo zaka zitatu.

18 Ndipo Rehabiamu anadzitengera mkazi Mahalati, mwana wamkazi wa Yerimoti mwana wa Davide, ndi wa Abihaili mwana wamkazi wa Eliabu mwana wa Jese;

19 ndipo anambalira ana, Yeusi, ndi Semariya, ndi Zahamu.

20 Ndi pambuyo pace anatenga Maaka mwana wamkazi wa Abisalomu; ndipo anambalira Abiya, ndi Atai, ndi Ziza, ndi Selomiti.

21 Ndipo Rehabiamu anakonda Maaka mwana wamkazi wa Abisalomu koposa akazi ace onse, ndi akazi ace ang'ono (pakuti adatenga akazi khumi mphambu asanu ndi atatu, ndi akazi ang'ono makumi asanu ndi limodzi, nabala ana amuna makumi awiri mphambu asanu ndi atatu, ndi ana akazi makumi asanu ndi limodzi).

22 Ndipo Rehabiamu anaika Abiya mwana wa Maaka akhale wamkuru, kalonga mwa abale ace; ndiko kuti adzamlonga ufumu.

23 Ndipo anacita mwanzeru, nabalalitsa ana ace amuna onse m'maiko onse a Yuda ndi Benjamini, ku midzi yonse yamalinga; nawapatsa cakudya cocuruka, nawafunira akazi ocuruka.

12

1 Ndipo kunacitika, utakhazikika ufumu wa Rehabiamu, nalimbika iye, anasiya cilamulo ca Yehova, ndi Aisrayeli onse pamodzi naye.

2 Ndipo Rehabiamu atakhala mfumu zaka zinai, Sisaki mfumu ya ku Aigupto anakwerera Yerusalemu, popeza iwo adalakwira Yehova.

3 Anakwera ndi magareta cikwi cimodzi mphambu mazana awiri, ndi apakavalo zikwi makumi asanu ndi limodzi, ndi anthu adadza naye kuturuka m'Aigupto ngosawerengeka, Alubi, Asuki, ndi Akusi.

4 Ndipo analanda midzi yamalinga yokhala ya Yuda, nadza ku Yerusalemu.

5 Pamenepo Semaya mneneri anadza kwa Rehabiamu, ndi kwa akalonga a Yuda, atasonkhana ku Yerusalemu cifukwa ca Sisaki, nati nao, Atero Yehova, Inu mwandisiya Ine, cifukwa cace Inenso ndasiya inu m'dzanja la Sisaki.

6 Pamenepo akalonga a Israyeli ndi mfumu anadzicepetsa, nati, Yehova ali wolungama.

7 Ndipo pamene Yehova anaona kuti anadzicepetsa, mau a Yehova anadza kwa Semaya, ndi kuti, Anadzicepetsa; sindidzawaononga; koma katsala kanthawi ndipo ndidzawapatsa cipulumutso, wosatsanulira mkwiyo wanga pa Yerusalemu ndi dzanja la Sisaki.

8 Koma adzakhala akapolo ace, kuti adziwe kunditumikira kwanga, ndi kuwatumikira kwa maufumu a maiko.

9 Ndipo Sisaki mfumu ya Aigupto anakwerera Yerusalemu, nacotsa cuma ca m'nyumba ya Yehova, ndi cuma ca m'nyumba ya mfumu; anazicotsa zonse; anacotsanso zikopa zagolidi adazipanga Solomo.

10 Ndipo Rehabiamu mfumu anapanga m'malo mwa izo zikopa zamkuwa, nazipereka m'manja mwa kapitao wa olindirira akusunga pakhomo pa nyumba ya mfumu.

11 Ndipo kunatero kuti pakulowa mfumu m'nyumba ya Yehova, anadza olindirira, nazinyamula, nazibwezanso ku cipinda ca olindirira.

12 Ndipo pakudzicepetsa iye mkwiyo wa Mulungu unamcokera, kuti usamuononge konse; ndiponso munatsalira zokoma m'Yuda.

13 Nadzilimbitsa Rehabiamu mfumu m'Yerusalemu, nacita ufumu; pakuti Rehabiamu anali wa zaka makumi anai mphambu cimodzi polowa ufumu wace, nakhala mfumu zaka khumi ndi zisanu ndi ziwiri m'Yerusalemu, ndiwo mudzi Yehova adausankha m'mafuko onse a Israyeli, kuikapo dzina lace; ndipo dzina la mace ndiye Naama M-amoni.

14 Koma anacita coipa, popeza sanalunjikitsa mtima wace kufuna Yehova.

15 Macitidwe ace tsono a Rehabiamu, zoyamba ndi zotsiriza, sizilembedwa kodi m'buku la mau a Semaya mneneriyo, ndi la Ido mlauliyo, lakunena za zibadwidwe? Ndipo panali nkhondo pakati pa Rehabiamu ndi Yerobiamu masiku onse.

16 Nagona Rehabiamu ndi makolo ace, naikidwa m'mudzi wa Davide; ndipo Abiya mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

13

1 Ndipo caka cakhumi mphambu zisanu ndi zitatu ca Yerobiamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda.

2 Anakhala mfumu m'Yerusalemu zaka zitatu; ndi dzina la mace ndiye Mikaya mwana wamkazi wa Uriyeli wa ku Gibeya. Ndipo panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yerobiamu.

3 Ndipo Abiya anayambana nkhondo ali ndi khamu la ngwazi za nkhondo, amuna osankhika zikwi mazana anai; Yerobiamu atandandalitsa nkhondo yace ilimbane naye ndi amuna osankhika zikwi mazana asanu ndi atatu, ndiwo ngwazi zamphamvu.

4 Ndipo Abiya anaimirira pa phiri la Zemaraimu, ndilo ku mapiri a Efraimu, nati, Mundimvere Yerobiamu ndi Aisrayeli onse;

5 simudziwa kodi kuti Yehova Mulungu wa Israyeli anapereka ciperekere ufumu wa Israyeli kwa Davide, kwa iye ndi ana ace, ndi pangano la mcere?

6 Koma Yerobiamu mwana wa Nebati mnyamata wa Solomo mwana wa Davide anauka, napandukana ndi mbuye wace.

7 Ndipo anamsonkhanira amuna acabe, anthu opanda pace, ndiwo anadzilimbikitsa kutsutsana naye Rehabiamu mwana wa Solomo, muja Rehabiamu anali mnyamata ndi woolowa mtima, wosakhoza kuwalaka.

8 Ndipo tsopano, mukuti mudzilimbikitse kutsutsana nao ufumu wa Yehova m'dzanja la ana a Davide; ndinu aunyinji ambiri, ndi pamodzi nanu ana a ng'ombe agolidi adawapanga Yerobiamu akhale milungu yanu.

9 Simunapitikitsa kodi ansembe a Yehova, ana a Aroni, ndi Alevi, ndi kudziikira ansembe monga amacita anthu a m'maiko ena? kuti ali yense wakudza kudzipatulira ndi mwana wa ng'ombe, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri, yemweyo ndiye wansembe wa iyo yosati milungu.

10 Koma ife, Yehova ndiye Mulungu wathu, sitinamsiya Iye; ndi ansembe tiri nao akutumikira Yehova ana a Aroni, ndi. Alevi, m'nchito mwao,

11 nafukizira Yehova nsembe zopsereza m'mawa ndi m'mawa, ndi madzulo onse, ndi zonunkhira za pfungo lokoma, nakonza mkate woonekera pa gome lopatulika, ndi coikapo nyali cagolidi ndi nyali zace, ziyake madzulo onse; pakuti tisunga cilangizo ca Yehova Mulungu wathu, koma inu mwamsiya Iye.

12 Ndipo taonani, Mulungu ali nafe, wotitsogolera ndi ansembe ace, ndi malipenga oliza nao cokweza, kukulizirani inu cokweza. Ana a Israyeli inu, musalimbane naye Yehova Mulungu wa makolo anu; pakuti simudzapindula nako.

13 Koma Yerobiamu anazunguliritsa owalalira, awadzere kumbuyo; momwemo iwowa anali kumaso kwa Yuda, ndi owalalira anali kumbuyo kwao.

14 Ndipo poceuka Yuda, taonani, nkhondo inayambana nao kumaso ndi kumbuyo; napfuulira iwo kwa Yehova, ndi ansembe analiza malipenga.

15 Pamenepo amuna a Yuda anapfuula cokweza; ndipo popfuula amuna a Yuda, kunacitika kuti Mulungu anakantha Yerobiamu ndi Aisrayeli onse pamaso pa Abiya ndi Yuda.

16 Ndipo ana a Israyeli anathawa pamaso pa Yuda, nawapereka Mulungu m'dzanja lao.

17 Ndipo Abiya ndi anthu ace anawakantha makanthidwe akuru; nagwa, nafa amuna osankhika zikwi mazanaasanu a Israyeli.

18 Momwemo anacepetsedwa ana a Israyeli nthawi ija, nalakika ana a Yuda; popeza anatama Yehova Mulungu wa makolo ao.

19 Ndipo Abiya analondola Yerobiamu, namlanda midzi yace, Beteli ndi miraga yace, ndi Yesana ndi miraga yace, ndi Efroni ndi miraga yace.

20 Ndi Yerobiamu sanaonanso mphamvu m'masiku a Abiya, namkantha Yehova, wa iye.

21 Koma Abiya anakula mphamvu, nadzitengera akazi khumi ndi anai, nabala ana amuna makumi awiri mphambu awiri, ndi ana akazi khumi mphambu asanu ndi mmodzi.

22 Macitidwe ena tsono a Abiya, ndi mayendedwe ace, ndi mau ace, alembedwa m'buku lomasulira la mneneri Ido.

14

1 Momwemo Abiya anagona ndi makolo ace, ndipo anamuika m'mudzi wa Davide; ndi Asa mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace, m'masiku ace dziko linaona bata zaka khumi.

2 Ndipo Asa anacita cokoma ndi coyenera m'maso mwa Yehova Mulungu wace,

3 nacotsa maguwa a nsembe acilendo, ndi misanje; naphwanya zoimiritsa zao, nalikha zifanizo zao,

4 nauza Yuda afune Yehova Mulungu wa makolo ao, ndi kucita cilamulo ndi cowauza, Iye.

5 Anacotsanso m'midzi yonse ya Yuda misanje, ndi zifanizo za dzuwa; ndi ufumuwo unacita bata pamaso pace.

6 Ndipo anamanga midzi yamalinga m'Yuda; pakuti dziko linacita bata, analibe nkhondo iyeyu zaka zija, popeza Yehova anampumulitsa.

7 Ndipo anati kwa Yuda, Timange midzi iyi ndi kuizingira malinga, ndi nsanja, zitseko, ndi mipiringidzo; dziko likali pamaso pathu, popeza tafuna Yehova Mulungu wathu; tamfuna Iye, natipatsa mpumulo pozungulira ponse. Momwemo anamanga mosabvutika.

8 Ndipo Asa anali nao ankhondo ogwira zikopa ndi mikondo, a m'Yuda zikwi mazana atatu; ndi a m'Benjamini ogwira malihawo ndi okoka mauta zikwi mazana awiri mphambu makumi asanu ndi atatu; onsewo ngwazi zamphamvu.

9 Ndipo anawaturukira Zera Mkusi ndi ankhondo zikwi cikwi cimodzi, ndi magareta mazana atatu; nafika iye ku Maresa.

10 Naturuka Asa pamaso pace, nanika nkhondoyi m'cigwa ca Sefata ku Maresa.

11 Ndipo Asa anapfuulira kwa Yehova Mulungu wace, nati, Yehova, palibe wina ngati Inu, kuthandiza pakati pa wamphamvu ndi iye wopanda mphamvu; tithandizeni Yehova Mulungu wathu, titama Inu, taturukira aunyinji awa m'dzina lanu. Yehova, Inu ndinu Mulungu wathu, munthu asakulakeni.

12 Ndipo Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Yuda, nathawa Akusi.

13 Ndi Asa ndi anthu anali naye anawalondola mpaka ku Gerari, nagwa Akusi ambiri osalimbikanso mphamvu iwowa; pakuti anathyoledwa pamaso pa Yehova ndi ankhondo ace; ndipo anatenga zofunkha zambiri.

14 Ndipo anakantha midzi yonse pozungulira pace pa Gerari; a pakuti mantha ocokera kwa Yehova anawagwera; ndipo anafunkha m'midzi monse, pakuti mudacuruka zofunkha m'menemo.

15 Anakanthanso a m'mahema a ng'ombe, nalanda nkhosa zocuruka, ndi ngamila; nabwerera kumka ku Yerusalemu.

15

1 Pamenepo mzimu wa Mulungu unagwera Azariya mwana wa Odedi,

2 ndipo anaturuka kukomana naye Asa, nanena naye, Mundimvere, Asa, ndi onse Ayuda ndi Abenjamini, Yehova ali nanu; mukakhala ndi Iye, mukamfuna Iye, mudzampeza; koma mukamsiya, adzakusiyani.

3 Masiku ambiri tsono Israyeli anakhala wopanda Mulungu woonayo, ndi wopanda wansembe wakuphunzitsa, ndi wopanda cilamulo;

4 koma pamene anatembenukira kwa Yehova Mulungu wa Israyeli m'kusautsidwa kwao, ndi kumfuna, anampeza.

5 Ndipo nthawi zija panalibe mtendere kwa iye wakuturuka, kapena kwa iye wakulowa, koma mabvuto akuru anagwera onse okhala m'maikomo.

6 Ndipo anapasulidwa, mtundu wa anthu kupasula unzace, ndi mudzi kupasula mudzi; pakuti Mulungu anawabvuta ndi masautso ali onse.

7 Koma limbikani inu, manja anu asalende; pakuti ku nchito yanu kuli mphotho.

8 Ndipo pakumva Asa mau awa, ndi cinenero ca Odedi mneneriyo, analimbika mtima, nacotsa zonyansazo m'dziko lonse la Yuda ndi Benjamini, ndi m'midzi adailanda ku mapiri a Efraimu; nakonza guwa la nsembe la Yehova lokhala pakhomo pa likole la Yehova.

9 Namemezaonse a m'Yuda ndi m'Benjamini, ndi iwo akukhala nao ocokera ku Efraimu, ndi Manase, ndi Simeoni; pakuti anamdzera ocuruka ocokera ku Israyeli, pamene anaona kuti Yehova Mulungu wace anali naye.

10 Ndipo anasonkhana ku Yerusalemu mwezi wacitatu, Asa atakhala mfumu zaka khumi ndi zinai.

11 Naphera Yehova nsembe tsiku lija za zofunkha adabwera nazo, ng'ombe mazana asanu ndi awiri, ndi nkhosa zikwi zisanu ndi ziwiri.

12 Nalowa cipangano cakufuna Yehova Mulungu wa makolo ao ndi mtima wao wonse, ndi moyo wao wonse;

13 ndi kuti yense wosafuna Yehova Mulungu wa Israyeli aphedwe, ngakhale wamng'ono kapena wamkuru, wamwamuna kapena wamkazi.

14 Ndipo analumbira kwa Yehova ndi mau akuru, ndi kupfuula ndi mphalasa ndi malipenga.

15 Ndipo Yuda yense anakondwera nalo lumbirolo; pakuti adalumbira ndi mtima wao wonse, namfunafuna ndi cifuno cao conse; ndipo anampeza; ndi Yehova anawapumulitsa pozungulirapo.

16 Maaka yemwe, mai wace wa Asa, mfumu, anamcotsa uyu asakhalenso mai wa ufumu, popeza anapanga fano loopsa la Asera; ndipo Asa analikha fano lace, naliphwanyaphwanya, nalitenthera ku mtsinje wa Kedroni.

17 Cinkana misanje siinacotsedwa m'Israyeli, mtima wa Asa unali wangwiro masiku ace onse.

18 Ndipo analowa nazo zopatulika za atate wace, ndi zopatulika zace zace, ku nyumba ya Mulungu; ndizo siliva, ndi golidi, ndi zipangizo.

19 Ndipo panalibenso nkhondo mpaka Asa atakhala mfumu zaka makumi atatu mphambu zinai.

16

1 Caka ca makumi atatu mphambu zisanu ndi cimodzi ca Asa, Basa mfumu ya Israyeli anakwera kulimbana ndi Yuda, namangitsa Rama, kuwaletsa anthu asaturuke kapena kulowa kwa Asa mfumu ya Yuda.

2 Pamenepo Asa anaturutsa siliva ndi golidi ku cuma ca nyumba ya Yehova, ndi ca nyumba ya mfumu; nazitumiza kwa Benihadadi mfumu ya Aramu, yokhala ku Damasiko, ndi kuti,

3 Pakhale pangano pakati pa ine ndi inu, monga pakati pa atate wange ndi atate wanu; taonani, ndakutumizirani siliva ndi golidi; mukani, pasulani pangano lanu ndi Basa mfumu ya Israyeli, kuti andicokere.

4 Ndipo Benihadadi anamvera mfumu Asa natumiza akazembe a magulu ace a nkhondo ayambane ndi midzi ya Israyeli, nakantha Iyoni, ndi Dani, ndi Abelimaimu, ndi midzi yonse ya cuma ya Nafitali,

5 Ndipo kunali, pakumva ici Basa, analeka kumangitsa Rama, naleketsa nchito yace.

6 Pamenepo Asa mfumu anatenga Ayuda onse, ndipo anatuta miyala ya ku Rama, ndi mitengo yace, imene Basa adamanga nayo, namangira Geba ndi Mizipa.

7 Nthawi yomweyi Hanani mlauli anadza kwa Asa mfumu ya Yuda, nanena naye, Popeza mwatama mfumu ya Aramu, osatama Yehova Mulungu wanu, cifukwa cace khamu la nkhondo la mfumu ya Aramu lapulumuka m'dzanja lanu.

8 Nanga Akusi ndi Alubi, sanakhala khamu lalikurukuru, ndi magareta ndi apakavalo ambirimbiri, koma muja munatama Yehova anawapereka m'dzanja mwanu?

9 Pakuti maso a Yehova ayang'ana uko ndi uko m'dziko lonse lapansi, kudzionetsera wamphamvu kwa iwo amene mtima wao uli wangwiro ndi Iye. Mwacita copusa m'menemo; pakuti kuyambira tsopano mudzaona nkhondo.

10 Koma Asa anakwiya naye mlauliyo, namuika m'kaidi; pakuti adapsa mtima naye cifukwa ca ici. Nthawi yomweyi Asa anasautsa anthu ena.

11 Ndipo taonani, zocita Asa, zoyamba ndi zotsiriza, zalembedwa m'buku la mafumu a Yuda ndi Israyeli.

12 Ndipo Asa atakhala mfumu zaka makumi atatu mpham bu zisanu ndi zitatu, anadwala nthenda ya mapazi, nikuladi nthendayi; koma podwala iye sanafuna Yehova, koma asing'anga.

13 Nagona Asa ndi makolo ace, namwalira atakhala mfumu zaka makumi anai.

14 Ndipo anamuika m'manda ace adadzisemerawo m'mudzi wa Davide, namgoneka pa kama wodzala ndi zonunkhira za mitundu mitundu, monga mwa makonzedwe a osanganiza; ndipo anampserezera zopsereza zambiri.

17

1 Ndipo Yehosafati mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace, nadzilimbitsa kuyambana ndi Israyeli.

2 Naika ankhondo m'midzi yonse yamalinga ya Yuda, naika aboma m'dziko la Yuda, ndi m'midzi ya Efraimu, imene adailanda Asa atate wace.

3 Ndipo Yehova anali ndi Yehosafati, popeza anayenda m'njira zace zoyamba za kholo lace Davide, osafuna Abaala;

4 koma anafuna Mulungu wa kholo lace nayenda m'malamulo ace, osatsata macitidwe a Israyeli.

5 Cifukwa cace Yehova anakhazikitsa ufumuwo m'dzanja lace, ndi onse Ayuda anabwera nayo mitulo kwa Yehosafati; ndipo zidamcurukira cuma ndi ulemu.

6 Ndi mtima wace unakwezeka m'njira za Yehova; anacotsanso misanje ndi zifanizo m'Yuda.

7 Caka cacitatu ca ufumu wace anatuma akalonga ace, ndiwo Benihayili, ndi Obadiya, ndi Zekariya, ndi Netaneli, ndi Mikaya, aphunzitse m'midzi ya Yuda;

8 ndi pamodzi nao Alevi, ndiwo Semaya, ndi Netaniya, ndi Zebadiya, ndi Asaheli, ndi Semiramoti, ndi Yonatani, ndi Adoniya, ndi Tobiya, ndi Tobadoniya, Alevi; ndi pamodzi nao Elisama ndi Yoramu, ansembe.

9 Ndipo anaphunzitsa m'Yuda ali nalo buku la cilamulo la Yehova, nayendayenda m'midzi yonse ya Yuda, naphunzitsa mwa anthu.

10 Ndipo kuopsa kwa Yehova kunagwera maufumu a maiko ozungulira Yuda; momwemo sanayambana ndi Yehosafati.

11 Ndipo Afilisti ena anabweca nazo kwa Yehosafati mitulo, ndi ndalama za msonkho; Aarabu omwe anabwera nazo kwa iye zoweta, nkhosa zamphongo zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu mazana asanu ndi awiri ndi atonde zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu mazana asanu ndi awiri.

12 Ndipo Yehosafati anakula cikulire, namanga m'Yuda nyumba zansanja, ndi midzi ya cuma.

13 Nakhala nazo nchito zambiri m'midzi ya Yuda, ndi anthu a nkhondo, ngwazi zamphamvu m'Yerusalemu.

14 Kuwerenga kwao monga mwa nyumba za atate ao ndiko: a Yuda, akuru a zikwi; Adina wamkuru, ndi pamodzi ndi iye ngwazi zamphamvu zikwi mazana atatu;

15 ndi wotsatana naye mkuru Yohanani, ndi pamodzi ndi iye zikwi mazana awiri mphambu makumi asanu ndi atatu;

16 ndi wotsatana naye Amasiya mwana wa Zikri, wodzipereka kwa Yehova mwaufulu, ndi pamodzi ndi iye ngwazi zamphamvu zikwi mazana awiri;

17 ndi a Benjamini: Eliyada ngwazi yamphamvu, ndi pamodzi ndi iye zikwi mazana awiri ogwira mauta ndi zikopa;

18 wotsatana naye Yozabadi, ndi pamodzi ndi iye okonzekeratu ku nkhondo zikwi zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu.

19 Ndiwo amene analindirira mfumu, osawerenga iwo aja mfumu adawaika m'midzi yamalinga m'Yuda monse.

18

1 Yehosafati tsono anali nacocuma ndi ulemu zomcurukira, nacita cibale ndi Ahabu.

2 Ndipo zitatha zaka zina, anatsikira kwa Ahabu ku Samariya. Ndi Ahabu anamphera iye ndi anthu anali naye nkhosa, ndi ng'ombe zocuruka; namnyenga akwere naye pamodzi ku Ramoti Gileadi.

3 Nati Ahabu mfumu ya Israyeli kwa Yehosafati mfumu ya Yuda, Mupita nane kodi ku Ramoti Gileadi? Nayankha, nati, Monga inu momwemo ine; monga anthu anu momwemo anthu anga; tidzakhala nanu ku nkhondoyi.

4 Ndipo Yehosafati anati kwa mfumu ya Israyeli, Funsiranitu mau a Yehova lero lino.

5 Pamenepo mfumu ya Israyeli anamemeza aneneri amuna mazana anai, nanena nao, Kodi timuke kunkhondo ku Ramoti Gileadi kapena ndileke? Ndipo anati, Kweraniko, pakuti Mulungu adzaupereka m'dzanja la mfumu.

6 Koma Yehosafati anati, Kulibenso kuno mneneri wa Yehova, kuti tifunsire kwa iye?

7 Ndipo mfumu ya Israyeli inati kwa Yehosafati, Atsalanso munthu mmodzi, tifunsire Yehova kwa iye; koma ndimuda, pakuti sandinenera ine kanthu kokoma, koma zoipa nthawi zonse, ndiye Mikaya mwana wa Yimla. Nati Yehosafati, Isatero mfumu.

8 Pamenepo mfumu ya Israyeli inaitana mdindo, niti, Katenge msanga Mikaya mwana wa Yimla.

9 Mfumu ya Israyeli tsono ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anakhala yense pa mpando wacifumu wace, obvala zobvala zacifumu zao, nakhala pamalo poyera polowera pa cipata ca Samariya; ndi aneneri onse ananenera pamaso pao.

10 Ndipo Zedekiya mwana wa Kenana anadzisulira nyanga zacitsulo, nati, Atero Yehova, Ndi izi udzagunda Aaramu mpaka adatha psiti.

11 Ndi aneneri onse ananenera momwemo, ndi kuti, Kwerani ku Ramoti Gileadi, mudzapindulako; pakuti Yehova adzaupereka m'dzanja la mfumu.

12 Ndipo mthenga wakukaitana Mikaya ananena naye, ndi kuti, Taonani, mau a aneneri anenera mfumu cokoma ngati m'kamwa m'modzi; mau anu tsono akhaletu ngati amodzi a iwowa, nimunene cokoma.

13 Nati Mikaya, Pali Yehova, conena Mulungu wanga ndidzanena comweci.

14 Pamene anafika kwa mfumu, mfumu inanena naye, Mikaya timuke ku Ramoti Gileadi kunkhondo kodi, kapena ndileke? Nati iye, Kwerani, mudzacita mwai; ndipo adzaperekedwa m'dzanja lanu.

15 Ndipo mfumu inati naye, Ndikulumbiritse kangati kuti unene nane coonadi cokha cokha m'dzina la Yehova?

16 Nati iye, Ndinaona Aisrayeli onse obalalika pamapiri ngati nkhosa zopanda mbusa; nati Yehova, Awa alibe mbuye wao, abwerere yense ku nyumba yace mumtendere.

17 Ndipo mfumu ya Israyeli inati kwa Yehosafati, Sindinakuuzani kuti sadzandinenera zabwino koma zoipa?

18 Nati iye, Cifukwa cace tamvani mau a Yehova, Ndinaona Yehova alikukhala pa mpando wace wacifumu, ndi khamu lonse lakumwamba lirikuima pa dzanja lace lamanja, ndi pa dzanja lace lamanzere.

19 Nati Yehova, Adzamnyenga Ahabu mfumu ya Israyeli ndani, kuti akwereko, nagwe ku Ramoti Gileadi? Nati wina mwakuti, wina mwakuti.

20 Ndipo unaturuka mzimu, nuima pamaso pa Yehova, nuti, Ndidzamnyenga ndine. Ndipo Yehova, ananena nao, Ndi ciani?

21 Nuti uwu, Ndidzaturuka ndi kukhala mzimu wonama m'kamwa mwa aneneri ace onse. Nati Iye, Udzamnyengadi, nudzakhoza; turuka, ukatero kumene.

22 Ndipo tsono taonani, Yehova analonga mzimu wabodza m'kamwa mwa aneneri anu awa, nakunenetserani coipa Yehova.

23 Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenana anayandikira, nampanda Mikaya patsaya, nati, Mzimu wa Yehova wandicokera bwanji kulankhula ndi iwe?

24 Nati Mikaya, Tapenya, udzaona tsiku lolowa iwe m'cipinda cam'kati kubisala.

25 Ndipo mfumu ya Israyeli inati, Mumtenge Mikaya, mukambweze kwa Amoni kazembe wa mudzi, ndi kwa Yoasi mwana wa mfumu;

26 nimuziti, Itero mfumu, Mumuike uyu m'kaidi, ndi kumdyetsa cakudya comsautsa, ndi kummwetsa madzi omsautsa, mpaka ndikabwera mumtendere.

27 Nati Mikaya, Mukakabwera ndi mtendere konse, Yehova sananena mwa ine. Natiiye, Tamverani, anthu inu nonsenu.

28 Momwemo mfumu ya Israyeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anakwera kumka ku Ramoti Gileadi.

29 Ndi mfumu ya Israyeli inati kwa Yehosafati, Ndidzadzizimbaitsa ndi kulowa kunkhondo, koma inu bvalani zobvala zanu. Nidzizimbaitsa mfumu ya Israyeli, namuka iwo kunkhondo.

30 Mfumu ya Aramu tsono idauza akapitao a magareta ace, ndi kuti, Musayambana ndi ang'ono kapena akuru, koma ndi mfumu ya Israyeli yekha.

31 Ndipo kunali, pamene akapitao a magareta anaona Yehosafati, anati, Ndiye mfumu ya Israyeli. Potero anamtembenukira kuyambana naye; koma Yehosafati anapfuula, namthandiza Yehova; ndipo Mulungu anawapambukitsa amleke.

32 Ndipo kunali, pamene akapitao a magareta anaona kuti sanali mfumu ya Israyeli anabwerera osamtsatanso.

33 Ndipo munthu anaponya mubvi wace ciponyeponye, namlasa pakati pa maluma a maraya ace acitsulo. Potero anati kwa woyendetsa garetayo, Tembenuza dzanja lako, nundicotse ku khamu la nkhondo kuno, pakuti ndalasidwa.

34 Ndipo nkhondo inakula tsiku lija; koma mfumu ya Israyeli inagwirizizil ka m'gareta wace popenyana ndi Aaramu mpaka madzulo, namwalira nthawi yakulowa dzuwa.

19

1 Ndipo Yehosafati mfumu ya Yuda anabwerera ku nyumba yace ku Yerusalemu mumtendere.

2 Naturuka Yehu mwana wa Hanani mlauli kukomana naye, nati kwa mfumu Yehosafati, Muyenera kodi kuthandiza oipa, ndi kukonda amene adana ndi Yehova? Cifukwa ca ici ukugwerani mkwiyo wocokera kwa Yehova.

3 Koma zapezeka zokoma mwa inu, popeza mwazicotsa zifanizo m'dzikomo, mwaluniikitsanso mtima wanu kufuna Mulungu.

4 Ndipo Yehosafati anakhala ku Yerusalemu, naturukiranso mwa anthu kuyambira ku Beereseba kufikira ku mapiri a Efraimu; nawabweza atsatenso Yehova Mulungu wa makolo ao.

5 Naika oweruza m'dziko, m'midzi yonse yamalinga ya m'Yuda, m'mudzi m'mudzi;

6 nati kwa oweruza, Khalani maso umo mucitira; pakuti simuweruzira anthu koma Yehova; ndipo ali nanu Iyeyu pakuweruza mlandu.

7 Ndipo tsono, kuopa Yehova kukhale pa inu, musamalire ndi kucita; pakuti palibe cosalungama kwa Yehova Mulungu wathu, kapena kusamalira monga mwa nkhope ya munthu, kapena kulandira mphatso.

8 Yehosafati anaikanso m'Yerusalemu Alevi, ndi ansembe ena, ndi akuru a nyumba za makolo m'Israyeli, aweruzire Yehova, nanene mirandu. Ndipo anabwerera kudza ku Yerusalemu.

9 Ndipo anawalangiza, ndi kuti, Muzitero ndi kuopa Yehova mokhulupirika ndi mtima wangwiro.

10 Ndipo ukakudzerani mlandu uli wonse wocokera kwa abale anu okhala m'midzi mwao, kusiyanitsa pakati pa mwazi ndi mwazi, pakati pa cilamulo ndi ciuzo, malemba ndi maweruzo, muwacenjeze kuti asaparamule kwa Yehova, angafikitsire inu nokha ndi abale anu mkwiyo; muzitero, ndipo simudzaparamula.

11 Ndipo taonani, Amariya wansembe wamkuru, ndiye mkuru wanu m'mirandu yonse ya Yehova; ndi Zebadiya mwana wa Ismayeli, wolamulira nyumba ya Yuda, m'mirandu yonse ya mfumu; ndi Alevi akhale akapitao pamaso panu. Citani molimbika mtima, ndipo Yehova akhale ndi abwino.

20

1 Ndipo zitatha izi, kunacitika kuti ana a Moabu, ndi ana a Amoni, ndi ena pamodzi ndi Aamoni, anadza kuyambana nkhondo ndi Yehosafati.

2 Pamenepo anadza anthu akuuza Yehosafati, kuti, Ukudzerani unyinji waukuru wa anthu ocokera tsidya la nyanja ku Aramu; ndipo taonani, ali ku Hazazoni Tamara, ndiwo Engedi.

3 Ndipo Yehosafati anacita mantha, nalunjikitsa nkhope yace kufuna Yehova, nalalikira kusala mwa Ayuda onse.

4 Namemezedwa Yuda afunsire kwa Yehova, inde anacokera ku midzi yonse ya Yuda kufuna Yehova.

5 Ndipo Yehosafati anaima mu msonkhano wa Ayuda, ndi a ku Yerusalemu, ku nyumba ya Yehova, pakati pa bwalo latsopano;

6 nati, Yehova Mulungu wa makolo athu, Inu sindinu Mulungu wa m'Mwamba kodi? sindinu woweruza maufumu onse a amitundu kodi? ndi m'dzanja mwanu muli mphamvu yolimba; palibe wina wakulaka Inu.

7 Sindinu Mulungu wathu, amene munainga nzika za m'dziko muno pa maso pa ana anu Israyeli, ndi kulininkha kwa mbeu ya Abrahamu bwenzi lanu kosatha?

8 nakhala m'mwemo iwowa, nakumangirani m'mwemo malo opatulika a dzina lanu, ndi kuti,

9 Cikatigwera coipa, lupanga, ciweruzo, kapena mliri, kapena njala, tidzakhala ciriri pakhomo pa nyumba iyi, ndi pamaso panu, (pakuti m'nyumba muno muli dzina lanu), ndi kupfuulira kwa Inu m'kusauka kwathu; ndipo mudzamvera ndi kulanditsa.

10 Ndipo tsopano, taonani ana a Amoni, ndi Moabu, ndi a ku phiri la Seiri, amene simunalola Israyeli awalowere, pakuturuka iwo m'dziko la Aigupto, koma anawapambukira osawaononga;

11 tapenyani, m'mene atibwezera; kudzatiinga m'colowa canu, cimene munatipatsa cikhale colowa cathu.

12 Mulungu wathu, simudzawaweruza? pakuti mwa ife mulibe mphamvu yakulimbana nao aunyinji ambiri awa akutidzera; ndipo sitidziwa ngati tidzatani, koma maso athu ali kwa Inu.

13 Ndipo Ayuda onse anakhala ciriri pamaso pa Yehova, pamodzi ndi makanda ao, akazi ao, ndi ana ao.

14 Pamenepo mzimu wa Yehova unagwera Yahazieli mwana wa Zekriya, mwana wa Benaya, mwana wa Yetieli, mwana wa Mataniya, Mlevi, wa ana a Asafu, pakati pa msonkhano;

15 nati iye, Tamverani Ayuda inu nonse, ndi inu okhala m'Yerusalemu, ndi inu mfumu Yehosafati, atero nanu Yehova, Musaope musatenge nkhawa cifukwa ca aunyinji ambiri awa; pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.

16 Mawa muwatsikire; taonani, akwera pokwerera pa Zizi, mudzakomana nao polekezera cigwa cakuno ca cipululu ca Yerueli.

17 Si kwanu kucita nkhondo kuno ai; cirimikani, imani, nimupenye cipulumutso ca Yehova pa inu Yuda ndi Yerusalemu; musaope, kapena kutenga nkhawa; mawa muwaturukire, popeza Yehova ali ndi inu.

18 Ndipo Yehosafati anawerama mutu wace, nkhope yace pansi; ndi Ayuda onse, ndi okhala m'Yerusalemu anagwa pansi pamaso pa Yehova, nalambira Yehova.

19 Ndipo Alevi, a ana a Akohati, ndi a ana a Kora, anauka kulemekeza Yehova Mulungu wa Israyeli ndi mau omveketsa.

20 Nalawira mamawa, naturuka kumka ku cipululu ca Tekoa; ndipo poturuka iwo, Yehosafati anakhala ciriri, nati, Mundimvere ine, Ayuda inu, ndi inu okhala m'Yerusalemu, Hmbikani mwa Yehova Mulungu wanu, ndipo mudzakhazikika; khulupirirani aneneri ace, ndipo mudzalemerera.

21 Ndipo atafunsana ndi anthu, anaika oyimbira Yehova, ndi kulemekeza ciyero cokometsetsa, pakuturuka iwo kutsogolera khamu la nkhondo, ndi kuti, Yamikani Yehova, pakuti cifundo cace cikhala cosatha.

22 Ndipo poyamba iwo kuyimba, ndi kulemekeza Yehova, anaika olalira alalire Aamoni, Amoabu, ndi a m'phiri la Seiri, akudzera Ayuda; ndipo anawakantha.

23 Pakuti ana a Amoni, ndi a Moabu, anaukira okhala m'phiri la Seiri, kuwapha ndi kuwaononga psiti; ndipo atatha okhala m'Seiri, anasandulikirana kuonongana.

24 Ndipo pofika Ayuda ku dindiro la kucipululu, anapenyera aunyinjiwo; taonani, mitembo iri ngundangunda, wosapulumuka ndi mmodzi yense.

25 Ndipo pofika Yehosafati ndi anthu ace kutenga zofunkha zao, anapezako cuma cambiri, ndi mitembo yambiri, ndi zipangizo zofunika, nadzifunkhira, osakhoza kuzisenza zonse; nalimkutenga zofunkhazo masiku atatu, popeza zinacuruka.

26 Ndi tsiku lacinai anasonkhana m'cigwa ca Beraka; pakuti pamenepo analemekeza Yehova; cifukwa cace anacha dzina lace la malowo, Cigwa ca Beraka, mpaka lero lino.

27 Pamenepo anabwerera amuna onse a Yuda, ndi a ku Yerusalemu, nawatsogolera ndi Yehosafati, kubwerera kumka ku Yerusalemu ndi cimwemwe; pakuti Yehova anawakondweretsa pa adani ao.

28 Ndipo anafika ku Yerusalemu ndi zisakasa, ndi azeze, ndi malipenga, ku nyumba ya Yehova.

29 Ndipo kuopsa kwa Mulungu kunagwera maufumu onse a m'maiko, pamene anamva kuti Yehova adayambana ndi adani a Israyeli.

30 Nucita bata ufumu wa Yehosafati; pakuti Mulungu wace anampumulitsira pozungulirapo.

31 Momwemo Yehosafati anakhala mfumu ya Yuda; anali wa zaka makumi atatu mphambu zisanu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi awiri; ndi dzina la mace ndiye Azuba mwana wa Sili.

32 Ndipo anayenda m'njira ya Asa atate wace osapambukamo, nacita zoongoka pamaso pa Yehova.

33 Komatu misanje siinacotsedwa; popeza pamenepo anthu sadakonzere mitima yao kwa Mulungu wa makolo ao.

34 Macitidwe ena tsono adazicita Yehosafati, zoyamba ndi zotsiriza, taonani, zilembedwa m'buku la mau a Yehu mwana wa Hanani, wochulidwa m'buku la mafumu a Israyeli.

35 Zitathaizi, Yehosafati mfumu ya Yuda anaphatikana ndi Ahaziya mfumu ya Israyeli, yemweyo anacita moipitsitsa;

36 naphatikana naye kupanga zombo zomuka ku Tarisi, nazipanga zombozo m'Ezioni Gebere.

37 Pamenepo Eliezeri mwana wa Dodavahu wa Maresa ananenera kumtsutsa Yehosafati, ndi kuti, Popeza waphatikana ndi Ahaziya Yehova wapasula nchito zako. Ndipo zombo zinasweka zosakhoza kumuka ku Tarisi.

21

1 Ndipo Yehosafati anagona pamodzi ndi makolo ace, naikidwa pamodzi ndi makolo ace m'mudzi wa Davide; ndi Yehoramu mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

2 Ndipo anali nao abale ace, ana a Yehosafati, Azariya, ndi Yehieli, ndi Zekariya, ndi Azariya, ndi Mikaeli, ndi Sefatiya, onsewa ndiwe ana a Yehosafati mfumu ya Israyeli.

3 Ndipo atate wao anawapatsa mphatso zazikuru, za siliva, ndi za golidi, ndi za mtengo wace, pamodzi ndi midzi yamalinga m'Yuda; koma ufumu anauninkha kwa Yehoramu; pakuti ndiye mwana wace woyamba.

4 Atauka tsono Yehoramu m'ufumu wa atate wace, nadzilimbitsa, anapha ndi lupanga abale ace onse, ndi akalonga ena omwe a Israyeli,

5 Yehoramu anali wa zaka makumi atatu mphambu ziwiri polowa ufumu wace, nacita ufumu m'Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.

6 Nayenda m'njira ya mafumu a Israyeli, umo anacitira nyumba ya Ahabu; pakuti mwana wamkazi wa Ahabu anali mkazi wace; ndipo anacita coipa pamaso pa Yehova.

7 Koma Yehova sanafuna kuononga nyumba ya Davide cifukwa ca pangano adalicita ndi Davide, ndi monga adalonjeza kumpatsa iye ndi ana ace nyali nthawi zonse.

8 Masiku ace Aedomu anapanduka kucoka m'dzanja la Yuda, nadziponyera okha mfumu.

9 Ndipo Yehoramu anaoloka, ndi akazembe ace, ndi magareta ace onse pamodzi naye, nauka usiku, nakantha Aedomu omzinga ndi akapitao a magareta,

10 Cinkana anatero, Aedomu anapanduka kupulumuka m'dzanja la Yuda mpaka lero lino; nthawi yomweyo anapanduka Alibina kupulumuka m'dzanja lace; cifukwa adasiya Yehova Mulungu wa makolo ace.

11 Anamanganso misanje m'mapiri a Yuda, nacititsa okhala m'Yerusalemu cigololo, nakankhirako Ayuda.

12 Ndipo anamdzera kalata wofuma kwa Eliya mneneri, ndi kuti, Atero Yehova Mulungu wa Davide atate wanu, Popeza simunayenda m'njira za Yehosafati atate wanu, kapena m'njira za Asa mfumu ya Yuda,

13 koma mwayenda m'njira ya mafumu a Israyeli, ndi kucititsa Yuda ndi okhala m'Yerusalemu cigololo, monga umo anacitira cigololo a nyumba ya Ahabu, mwaphanso abale anu a nyumba ya atate wanu, ndiwo abwino akuposa inu;

14 taonani, Yehova adzakantha anthu anu, ndi ana anu, ndi akazi anu, ndi cuma canu conse, makanthidwe akuru;

15 ndipo mudzadwala kwakukuru nthenda yamatumbo, mpaka matumbo anu adzaturuka cifukwa ca nthendayi tsiku ndi tsiku.

16 Ndipo Yehova anautsira Yehoramu mzimu wa Afilisti, ndi wa Aarabu okhala pambali pa Akusi;

17 ndiwo anakwerera Yuda, nathyolamo, nalanda cuma conse cinapezeka m'nyumba ya mfumu, ndi ana ace omwe, ndi akazi ace, osamsiyira mwana, koma Yehoahazi yekha mwana wace wamng'ono.

18 Ndi pambuyo pace pa izi zonse Yehova anamdwalitsa m'matumbo ace ndi nthenda yosacira nayo.

19 Ndipo kunali, itapita nthawi, pakutha pace pa zaka ziwiri, anaturuka matumbo ace mwa nthenda yace namwalira nazo nthenda zoipa, Ndipo anthu ace sanampserezera zonunkhira, monga umo anapserezera makolo ace.

20 Anali wa zaka makumi atatu mphambu ziwiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu, namuka wopanda wina womlakalaka; ndipo anamuika m'mudzi wa Davide, koma si m'manda a mafumu ai.

22

1 Ndipo okhala m'Yerusalemu anamlonga Ahaziya mwana wace wamng'ono akhale mfumu m'malo mwace; pakuti gulu la anthu, adadzawo pamodzi ndi Aarabu kucigono, adapha ana oyamba onse. Momwemo Ahaziya mwana wa Yehosafati anakhala mfumu ya Yuda.

2 Ahaziya anali wa zaka makumi anai mphambu ziwiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu caka cimodzi; ndi dzina la mace ndiye Ataliya mwana wa Omri.

3 Iyenso anayenda m'njira za nyumba ya Ahabu; pakuti wompangira ndi mace acite coipa,

4 Ndipo anacita coipa pamaso pa Yehova, monga umo anacitira a nyumba ya Ahabu; pakuti ompangira ndi iwowa, atamwalira atate wace; ndi kuonongeka kwace nkumeneko.

5 Anayendanso m'kupangira kwao, namuka pamodzi ndi Yehoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israyeli, kukayambana nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Gileadi; ndipo Aaramu anamlasa Yehoramu.

6 Nabwerera iye kuti amcize ku Yezreeli, apole mabala amene adamkantha ku Rama, pamene anayambana ndi Hazaeli mfumu ya Aramu, Ndipo Azariya mwana wa Yehoramu mfumu yaYuda anatsikira kukaona Yehoramu mwana wa Ahabu m'Yezreeli, popeza anadwala.

7 Kuonongeka kwa Ahaziya tsono nkwa Mulungu, kuti amuke kwa Yehocamu; pakuti atafika anaturukira pamodzi ndi Yehoramu kukayambana ndi Yehu mwana wa Nimsi, amene Yehova anamdzoza alikhe nyumba ya Ahabu.

8 Ndipo kunali, pakulanga Yehu nyumba ya Ahabu, anapeza akalonga a Israyeli, ndi ana a abale a Ahaziya, akutumikira Ahaziya, nawapha.

9 Atatero, anafunafuna Ahaziya, namgwira alikubisala m'Samariya, nabwera naye kwa Yehu, namupha; ndipo anamuika; pakuti anati, Ndiye mwana wa Yehosafati, wofuna Yehova ndi mtima wace wonse. Ndipo panalibe wina wa nyumba ya Ahaziya wa mphamvu yakusunga ufumuwo.

10 Pamene Ataliya anaona kuti mwana wace adafa, anauka, naononga mbeu yonse yacifumu ya nyumba ya Yuda.

11 Koma Yehosafati mwana wamkazi wa mfumu anatenga Yoasi mwana wa Ahaziya, namuba pakati pa ana a mfumu ophedwa, namlonga iye ndi mlezi wace m'cipinda cogonamo. Momwemo Yehosafati mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, mkazi wa Yehoyada wansembe (popeza ndiye mlongo wace wa Ahaziya), anambisira Ataliya, angamuphe.

12 Ndipo iye anali nao wobisika m'nyumba ya Mulungu zaka zisanu ndi cimodzi; nakhala Ataliya mfumu yaikazi ya dziko.

23

1 Koma caka cacisanu ndi ciwiri Yehoyada anadzilimbitsa natenga atsogoleri a mazana, Azariya mwana wa Yeroamu, ndi Ismayeli mwana wa Yohanana, ndi Azariya mwana wa Obedi, ndi Maaseya mwana wa Adaya, ndi Elisafati mwana wa Zikiri, apangane naye pamodzi.

2 Ndipo iwo anayendayenda mwa Yuda, nasonkhanitsa Alevi m'midzi yonse ya Yuda, ndi akuru a nyumba za makolo m'Israyeli; nadza iwo ku Yerusalemu.

3 Ndipo msonkhano wonse unapangana pangano ndi mfumu m'nyumba ya Mulungu. Ndipo ananena nao, Taonani, mwana wa mfumu adzakhala mfumu monga Yehova ananena za ana a Davide.

4 Cimene muzicita ndi ici: limodzi la magawo atatu mwa inu olowera dzuwa la Sabata, la ansembe ndi Alevi, akhale olindirira pakhomo;

5 ndi limodzi la magawo atatu likhale ku nyumba ya mfumu; ndi limodzi la magawo atatu ku cipata ca maziko; ndi anthu onse akhale m'mabwalo a nyumba ya Yehova.

6 Koma asalowe mmodzi m'nyumba ya Yehova, ansembe okha, ndi Alevi otumikira, alowe iwowa; pakuti ndiwo opatulika; koma anthu onse asunge udikiro wa Yehova.

7 Ndipo Alevi amzinge mfumu pozungulirapo, yense ndi zida zace m'dzanja mwace; ndipo ali yense wolowa m'nyumba aphedwe; nimukhale inu pamodzi ndi mfumu pakulowa ndi pakuturuka iye.

8 Momwemo Alevi ndi Ayuda onse anacita monga mwa zonse anawauza Yehoyada wansembe; natenga yense amuna ace alowe dzuwa la Sabata pamodzi ndi oturuka dzuwa la Sabata; pakuti Yehoyada wansembe sanamasula zigawo.

9 Ndi Yehoyada wansembe anapereka kwa akazembe a mazana mikondo, ndi zikopa, ndi maraya acitsulo, zinali za mfumu Davide, zokhala m'nyumba, ya Mulungu.

10 Ndipo anaika anthu onse, yense ndi cida cace m'dzanja lace, amzinge mfumu, kuyambira mbali ya ku dzanja lamanja la nyumba kufikira mbali ya ku dzanja lamanzere la nyumba, kuloza ku guwa la nsembe ndi kunyumba.

11 Pamenepo anaturutsa mwana wa mfumu, nambveka korona, nampatsa mboni, namlonga ufumu; ndi Yehoyada ndi ana ace anamdzoza, nati, Ikhale ndi moyo mfumu.

12 Ndipo pamene Ataliya anamva phokoso la anthu alikuthamanga ndi kulemekeza mfumu, anadza kwa anthu m'nyumba ya Yehova;

13 napenya, ndi kuona mfumu inaima pa nsanamira yace polowera; ndi atsogoleri, ndi malipenga, anali kwa mfumu; ndi anthu onse a m'dziko anakondwera, naomba amalipenga; oyimbira omwe analiko ndi zoyimbirazo, nalangiza poyimbira colemekeza. Pamenepo Ataliya anang'amba zobvala zace, nati, Ciwembu, ciwembu.

14 Koma Yehoyada wansembe anaturuka nao atsogoleri a mazana akuyang'anira khamu la nkhondo, nanena nao, Mturutseni mkaziyo pakati pa mipambo; ndipo ali yense womtsata aphedwe ndi lupanga; pakuti wansembe adati, Msamphere m'nyumba ya Yehova.

15 Ndipo anampisa malo; namuka iye kolowera ku cipata ca akavalo kunyumba ya mfumu; ndi pomwepo anamupha.

16 Ndipo Yehoyada anacita pangano pakati pa iye, ndi anthu onse, ndi mfumu, kuti adzakhala anthu a Yehova.

17 Ndi anthu onse anamuka ku nyumba ya Baala, naipasula, naphwanya maguwa ace a nsembe, ndi mafano ace; namupha Matana wansembe wa Baala ku maguwa a nsembe.

18 Ndipo Yehoyada anaika mayang'aniro a nyumba ya Yehova m'dzanja la ansembe Aleviwo, amene Davide anawagawa, ayang'anire nyumba ya Yehova; napereka nsembe zopsereza za Yehova monga mulembedwa m'cilamulo ca Mose, ndi kukondwera ndi kuyimbira, monga mwa cilangizo ca Davide.

19 Ndipo anaika odikira ku makomo a nyumba ya Yehova, kuti wodetsedwa nako kanthu kali konse asalowemo.

20 Natenga atsogoleri a mazana, ndi omveka, ndi akazembe a anthu, ndi anthu onse a m'dziko, natsika ndi mfumu ku nyumba ya Yehova; nalowera pa cipata ca kumtunda m'nyumba ya mfumu, namkhalitsa mfumu pa mpando wa ufumu.

21 Ndipo anthu onse a m'dziko anakondwera; ndi m'mudzi munali cete, atamupha Ataliya ndi lupanga.

24

1 Yoasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi anai; ndi dzina la mace ndiye Zibiya wa ku Beereseba.

2 Ndipo Yoasi anacita zoongoka pamaso pa Yehova masiku onse a Yehoyada wansembe.

3 Ndipo Yehoyada anamtengera akazi awiri, nabala ana amuna ndi akazi.

4 Ndipo pambuyo pace mumtima mwa Yoasi munali cofuna kukonzanso nyumba ya Yehova.

5 Nasonkhanitsa ansembe ndi Alevi, nanena nao, Muturuke kumka ku midzi ya Yuda, ndi kusonkhanitsa kwa Aisrayeli onse ndarama zakukonzetsa nyumba ya Mulungu wanu caka ndi caka; ndipo inu fulumirani nayo nchitoyi. Koma Alevi sanafulumira nayo.

6 Ndipo mfumu inaitana Yehoyada mkuru wao, niti naye, Unalekeranji kuuza Alevi abwere nao kucokera m'Yuda ndi Yerusalemu msonkho wa Mose mtumiki wa Yehova, ndi wa msonkhano wa Israyeli, ukhale wa cihema ca umboni?

7 Pakuti ana a Ataliya mkazi woipa uja anathyola citseko ca nyumba ya Mulungu, natenga zopatulidwa zonse za nyumba ya Yehova kuzipereka kwa Baala.

8 Nilamulira mfumu, ndipo anapanga bokosi, naliika kunja ku cipata ca nyumba ya Yehova.

9 Nalalikira mwa Yuda ndi Yerusalemu, abwere nao kwa Yehova msonkho umene Mose mtumiki wa Mulungu anauikira Aisrayeli m'cipululu.

10 Ndipo akalonga onse ndi anthu onse anakondwera, nabwera nazo, naponya m'bokosi mpaka atatha.

11 Ndipo kunali, pamene amabwera nalo bokosi alipenye mfumu, mwa manja a Alevi, nakapenya kuti ndalama zinacurukamo, amadza mlembi wa mfumu, ndi kapitao wa wansembe wamkulu, nakhutula za m'bokosi, nalisenza ndi kubwera nalo kumalo kwace. Anatero tsiku ndi tsiku, nasonkhanitsa ndalama zocuruka.

12 Ndipo mfumu ndi Yehoyada anazipereka kwa iwo akugwira nchito ya utumiki ya nyumba ya Yehova, nalembera amisiri omanga ndi miyala, ndi osema mitengo, akonzenso nyumba ya Yehova; ndiponso akucita ndi citsulo ndi mkuwa alimbitse nyumba ya Yehova.

13 Momwemo anacita ogwira nchito, nikula nchito mwa dzanja lao, nakhazikitsa iwo nyumba ya Mulungu monga mwa maonekedwe ace, nailimbitsa.

14 Ndipo ataitsiriza, anabwera nazo ndalama zotsala kwa mfumu ndi Yehoyada, napanga nazo zipangizo za nyumba ya Yehova, zipangizo za kutumikira nazo, ndi kupereka nsembe nazo, ndi zipande, ndi zipangizo za golidi ndi siliva. Ndipo anapereka kosalekeza nsembe zopsereza m'nyumba ya Yehova masiku onse a Yehoyada.

15 Koma Yehoyada anakalamba, nacuruka masiku, namwalira iye; ndiye wa zaka zana limodzi mphambu makumi atatu pamene anamwalira.

16 Ndipo anamuika m'mudzi wa Davide, pakati pa mafumu; pakuti anacita zabwino m'Israyeli, ndi kwa Mulungu, ndi ku nyumba yace.

17 Atamwalira Yehoyada tsono, akalonga a Yuda anadza, nalambira mfumu. Ndipo mfumu inawamvera.

18 Ndipo anasiya nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo ao, natumikira zifanizo, ndi mafano; ndipo mkwiyo unawagwera Yuda ndi Yerusalemu, cifukwa ca kuparamula kwao kumene.

19 Koma Iye anawatumira aneneri kuwabwezeranso kwa Yehova, ndiwo anawacitira umboni; koma sanawamvera.

20 Ndipo mzimu wa Mulungu unabvala Zekariya mwana wa Yehoyada wansembe, naima iye kumtunda kwa anthu, nanena nao, Atero Mulungu, Mulakwiranji malamulo a Yehova kuli kosalemerera nako? Popeza mwasiya Yehova, Iye wasiyanso inu.

21 Koma anampangira ciwembu, namponya miyala, mwa lamulo la mfumu m'bwalo la nyumba ya Yehova.

22 Motero mfumu Yoasi sanakumbukila zokoma anamcitirazi Yehoyada atate wace, koma anapha mwana wace; ndiye pomwalira anati, Yehova acipenye, nacifunse.

23 Ndipo kunacitika, podzanso nyengoyi khamu la nkhondo la Aaramu linamkwerera, nafika iwo ku Yuda ndi Yerusalemu, naononga mwa anthu akalonga onse a anthu, natumiza zofunkha zao zonse kwa mfumu ya ku Damasiko.

24 Pakuti khamu la nkhondo la Aaramu linadza la anthu owerengeka; ndipo Yehova anapereka khamu lalikuru m'dzanja lao; popeza adasiya Yehova Mulungu wa makolo ao. Motero anacitira Yoasi zomlanga.

25 Ndipo atamcokera (popeza anamsiya wodwala nthenda zazikuru), anyamata ace anamcitira ciwembu, cifukwa ca mwazi wa ana a Yehoyada wansembe, namupha pakama pace, namwalira iye; ndipo anamuika m'mudzi wa Davide, koma osamuika m'manda a mafumu.

26 Omcitira ciwembu ndi awa: Zabadi, mwana wa Simeati wamkazi M-amoni; ndi Yozabadi, mwana wa Simiriti wamkazi Mmoabu.

27 Za ana ace tsono, ndi katundu wamkuru anamsenza, ndi kumanganso kwa nyumba ya Mulungu, taonani, zilembedwa m'buku lomasulira la mafumu. Ndipo Amaziya mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

25

1 Amaziya anali wa zaka makumi awiri mphambu zisanu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi awiri mphambu zisanu ndi zinai; ndi dzina la mace ndiye Yehoadana wa ku Yerusalemu.

2 Ndipo anacita zoongoka pamaso pa Yehova, koma wosacita ndi mtima wangwiro.

3 Kunacitika tsono, utamkhazikikira ufumu, anapha anyamata ace amene adapha mfumu atate wace.

4 Koma sanapha ana ao, koma anacita monga umo mulembedwa m'cilamulo, m'buku la Mose, monga Yehova analamulira, ndi kuti, Atate asafere ana, ndi ana asafere atate; koma yense afere chimo lace lace.

5 Ndipo Amaziya anamemeza Ayuda, nawaika monga mwa nyumba za atate ao, atsogoleri a zikwi, ndi atsogoleri a mazana, ndiwo onse a Yuda ndi Benjamini; nawawerenga a zaka makumi awiri ndi mphambu, nawapeza amuna osankhika zikwi mazana atatu akuturukira kunkhondo, ogwira mkondo ndi cikopa.

6 Analemberanso ngwazi zamphamvu za m'Israyeli zikwi zana limodzi, kuwalipira matalente a siliva zana limodzi.

7 Koma anamdzera munthu wa Mulungu, kuti, Mfumu, khamu la nkhondo la Israyeli lisapite nanu; pakuti Yehova sakhala ndi Israyeli, sakhala ndi ana onse a Efraimu.

8 Koma ngati mumuka, citani, limbikani kunkhondo, Mulungu adzakugwetsani pamaso pa adani; pakuti Mulungu ali nayo mphamvu yakuthandiza ndi yakugwetsa.

9 Ndipo Amaziya anati kwa munthu wa Mulungu, Koma nanga titani nao matalente zana limodzi ndinapatsa ankhondo a Israyeli? Nati munthu wa Mulungu, Yehova ali nazo zoposa izi kukupatsani.

10 Pamenepo Amaziya anawapambutsa, ndiwo ankhondo anamdzera kucokera ku Efraimu, amuke kwao; potero adapsa mtima kwambiri pa Yuda, nabwera kwao ndi kutentha mtima.

11 Nalimbika mtima Amaziya, natsogolera anthu ace, namuka ku Cigwa ca Mcere, nakantha ana a Seiri zikwi khumi.

12 Ndi ana a Yuda anagwira zikwi khumi ena amoyo, nabwera nao pamwamba pa thanthwe, nawakankha pamwamba pa thanthwe, naphwanyika onsewo.

13 Koma amuna a nkhondo amene Amaziya anawabwereretsa, kuti asamuke naye kunkhondo, anagwera midzi ya Yuda kuyambira Samariya kufikira Betihoroni, nakantha a iwowa zikwi zitatu, nalanda zofunkha zambiri.

14 Ndipo kunali, atafika Amaziya atatha kuwapha Aedomu, ndi kubwera nayo milungu ya ana a Seiri, anaiika ikhale milungu yace, naigwadira, naifukizira,

15 Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unayakira Amaziya, ndipo anamtumira mneneri amene anati, Mwafuniranji milungu ya anthu imene siinalanditsa anthu ao m'dzanja lanu?

16 Ndipo kunali, pakulankhula naye mfumu, inanena naye, Takuika kodi ukhale wopangira mfumu? leka, angakukanthe. Pamenepo mneneriyo analeka, nati, Ndidziwa kuti Mulungu watsimikiza mtima kukuonongani, popeza mwacita ici ndi kusamvera kupangira kwanga.

17 Pamenepo Amaziya mfumu ya Yuda anafunsana ndi ompangira, natumiza kwa Yoasi mwana wa Yehoahazi mwana wa Yehu mfumu ya Israyeli, ndi kuti, Idzani, tionane maso.

18 Ndi Yoasi mfumu ya Israyeli anatumiza kwa Amaziya mfumu ya Yuda ndi kuti, Mtungwi wa ku Lebano unatumiza kwa mkungudza wa ku Lebano, ndi kuti, Mpatse mwana wanga wamwamuna mwana wako wamkazi akhale mkazi wace; koma nyama ya kuthengo ya ku Lebano inapitapo, nipondereza mtungwi.

19 Mukuti, Taonani, ndakantha Aedomu, nukwezeka mtima wanu kudzikuza; khalani kwanu tsopano, mungadziutsire tsoka, mungagwe, inu, ndi Yuda pamodzi ndi inu.

20 Koma wosamvera Amaziya, pakuti nca Mulungu ici kuti awapereke m'dzanja la adani ao; popeza anafuna milungu ya Edomu.

21 Motero anakwera Yoasi mfumu ya Israyeli, ndipo iye ndi Amaziya mfumu ya Yuda anapenyana maso ku Betisemesi, ndiwo wa Yuda.

22 Nakanthidwa Yuda pamaso pa Israyeli, nathawa yense kuhema kwace.

23 Ndipo Yoasi mfumu ya Israyeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yoasi mwana wa Yehoahazi, ku Betisemesi, nabwera naye ku Yerusalemu, nagamula linga la Yerusalemu kuyambira cipata ca Efraimu kufikira cipata ca kungondya, mikono mazana anai.

24 Natenga golidi ndi siliva zonse, ndi zipangizo zonse zopezeka m'nyumba ya Mulungu kwa Obedi Edomu, ndi cuma ca nyumba ya mfumu, acikole omwe; nabwerera kumka ku Samariya.

25 Ndipo Amaziya mwana wa Yoasi mfumu ya Yuda anakhala ndi moyo, atamwalira Yoasi mwana wa Yehoahazi mfumu ya Israyeli, zaka khumi ndi zisanu.

26 Macitidwe ena tsono a Amaziya, oyamba ndi otsiriza, taonani, salembedwa kodi m'buku la mafumu a Yuda ndi Israyeli?

27 Ndipo cipambukire Amaziya kusatsata Yehova, anamcitira ciwembu m'Yerusalemu, nathawira ku Lakisi iyeyu; koma anatuma omtsatira ku Lakisi, namupha komweko.

28 Namnyamula pa akavalo, namuika pamodzi ndi makolo ace m'mudzi wa Yuda.

26

1 Ndipo anthu onse Ayuda anatenga Uziya, ndiye wa zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi, namlonga ufumu m'malo mwa atate wace Amaziya.

2 Iye anamanga Eloti, naubweza kwa Yuda, mfumu itagona ndi makolo ace.

3 Uziya anali wa zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi asanu mphambu ziwiri; ndi dzina la mace ndiye Yekoliya wa ku Yerusalemu.

4 Nacita iye zoongoka pamaso pa Yehova, monga mwa zonse adazicita atate wace Amaziya.

5 Ndipo iye anali munthu wakufuna Mulungu masiku a Zekariya, ndiye wozindikira masomphenya a Mulungu; ndipo masiku akufunira Yehova iye, Mulungu anamlemereza;

6 popeza anaturuka, nayambana ndi Afilisti, nagamula linga la Gati, ndi linga la Yabine, ndi linga la Asidodi; namanga midzi m'dziko la Asidodi, ndi mwa Afilisti.

7 Ndipo Mulungu anamthandiza poyambana ndi Afilisti, ndi Aarabu okhala m'Guribaala, ndi Ameuni.

8 Ndipo Aamoni anampatsa Uziya mitulo; ndi dzina lace linabuka mpaka polowera ku Aigupto; pakuti analil mbika cilimbikire.

9 Uziya anamanganso nsanja m'Yerusalemu pa cipata ca kungondya, ndi pa cipata ca kucigwa, ndi popindika linga; nazilimbikitsa.

10 Namanga nsanja m'cipululu, nakumba zitsime zambiri; popeza anali nazo zoweta zambiri; kumadambo, ndi kuzidikha; nakhala nao olima minda, ndi osunga mpesa kumapiri ndi ku nthaka yopatsa bwino; pakuti ndiye mlimi.

11 Uziya anali nalonso khamu la anthu a nkhondo, oturuka kunkhondo magulu; nawawerenga monga mwa mawerengedwe ao ndi dzanja la mlembi Yeyeli, ndi kapitao Maseya, monga anawauza Hananiya kazembe wina wa mfumu.

12 Ciwerengo conse ca akuru a nyumba za makolo, ndiwo ngwazi zamphamvu, ndico zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi limodzi.

13 Ndipo m'dzanja mwao munali khamu la nkhondo zikwi mazana atatu mphambu zikwi zisanu ndi ziwiri kudza mazana asanu ocita nkhondo ndi mphamvu yaikuru, kuthandiza mfumu alimbane ndi adani.

14 Ndipo Uziya anawakonzeratu ankhondo onse zikopa, ndi mikondo, ndi zisoti zacitsulo, ndi maraya acitsulo, ndi mauta, ndi miyala yoponyera.

15 Napanga m'Yerusalemu makina, opangidwa ndi eni luso, akhale pansanja ndi kungondya, aponye nao mibvi ndi miyala yaikuru. Ndi dzina lace linamveka kutali; pakuti anathandizidwa modabwiza, mpaka analimbikatu.

16 Koma atakhala wamphamvu, mtima wace unakwezeka momuononga, nalakwira Yehova Mulungu wace; popeza analowa m'Kacisi wa Yehova kufukiza pa guwa la nsembe la cofukiza.

17 Ndipo Azariya wansembe analowa pambuyo pace, ndi pamodzi naye ansembe a Yehova makumi asanu ndi atatu, ndiwo olimba mtima;

18 natsutsana ndi mfumu Uziya, nati kwa iye, Sikuyenera inu, Uziya, kufukizira Yehova, koma ansembe, ana a Aroni opatulidwira kufukiza; turukani m'malo opatulika; pakuti mwalakwa; Yehova Mulungu sakulemekezanipo.

19 Koma Uziya anapsa mtima, mbale ya zofukiza iri m'dzanja lace kufukiza nayo; ndipo pakupsa mtima nao ansembe, khate linabuka pamphumi pace, pamaso pa ansembe m'nyumba ya Yehova, pambali pa guwa lofukizapo.

20 Ndipo Azariya wansembe wamkulu, ndi ansembe onse, anampenya, ndi kuona kuti anali wakhate pamphumi pace namkankhiza msanga kubwalo; nafulumiranso yekha kuturukako, pakuti Yehova adamkantha.

21 Ndipo mfumu Uziya anali wakhate mpaka tsiku la imfa yace, nakhala m'nyumba ya padera, popeza ndiye wakhate; pakuti anadulidwa ku nyumba ya Yehova; ndi Yotamu mwana wace anayang'anira nyumba ya mfumu naweruza anthu a m'dziko.

22 Macitidwe ena tsono a Uziya, oyamba ndi otsiriza, anawalemba Yesaya mneneri mwana wa Amosi. Ndipo Uziya anagona ndi makolo ace, namuika ndi makolo ace kumanda kwa mafumu; pakuti anati, Ndiye wakhate; ndi Yotamu mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

27

1 Yotamu anali wa zaka makumi awiri, mphambu zisanu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka khumi ndi zisanu ndi cimodzi; ndi dzina la mace ndiye Yerusa mwana wa Zadoki.

2 Ndipo anacita zoongoka pamaso pa Yehova, monga umo adacitira atate wace Uziya; pokhapo sanalowa m'Kacisi wa Yehova. Koma anthu anacitabe zobvunda.

3 Anamanga cipata ca kumtunda ca nyumba ya Yehova, ndi pa linga la Ofeli anamanga kwakukuru.

4 Namanga midzi m'mapiri a Yuda, ndi m'nkhalango anamanga nyumba zansanja, ndi nsanja zomwe.

5 Anayambananso ndi mfumu ya ana a Amoni, namgonjetsa, Ndi ana a Amoni anamninkha caka comweci matalente a siliva zana limodzi, ndi miyeso ya tirigu zikwi khumi, ndi ya barele zikwi khumi. Ana a Amoni anabwera nazo zomwezo kwa iye caka caciwiri ndi cacitatu comwe.

6 Momwemo Yotamu anakula mphamvu, popeza anakonza njira zace pamaso pa Yehova Mulungu wace.

7 Macitidwe ena tsono a Yotamu, ndi nkhondo zace zonse, ndi njira zace, taonani, zalembedwa m'buku la mafumu a Israyeli ndi Yuda.

8 Anali wa zaka makumi awiri mphambu zisanu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi.

9 Ndipo Yotamu anagona ndi makolo ace, namuika m'mudzi wa Davide; ndi Ahazi mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

28

1 Ahazi anali wa zaka makumi awiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka khumi mphambu zisanu ndi cimodzi; koma sanacita zoongoka pamaso pa Yehova ngati Davide kholo lace,

2 koma anayenda m'njira za mafumu a Israyeli, napangiranso Abaala mafano oyenga,

3 Nafukizanso yekha m'cigwa ca mwana wa Hinomu, napsereza ana ace m'moto, monga mwa zonyansa za amitundu, amene Yehova anawainga pamaso pa ana a Israyeli.

4 Naphera nsembe, nafukiza kumisanje, ndi kuzitunda, ndi patsinde pa mtengo uli wonse wogudira.

5 Cifukwa cace Yehova Mulungu wace anampereka m'dzanja la mfumu ya Aramu; ndipo anamkantha, natenga ndende unyinji waukuru wa anthu ace, nafika nao ku Damasiko. Anaperekedwanso iye m'dzanja la mfumu ya Israyeli, amene anamkantha makanthidwe akuru.

6 Pakuti Peka mwana wa Remaliya anapha ku Yuda tsiku limodzi zikwi zana limodzi ndi makumi awiri, ngwazi zonsezo; popeza adasiya Yehova Mulungu wa makolo ao.

7 Ndipo Zikiri munthu wamphamvu wa Efraimu anapha Maseya mwana wa mfumu, ndi Azrikamu woyang'anira nyumba, ndi Elikana wotsatana ndi mfumu.

8 Ndipo ana a Israyeli anatenga ndende ena a abale ao zikwi mazana awiri, akazi, ana amuna ndi akazi, nalandanso kwa iwo zofunkha zambiri, nabwera nazo zofunkhazo ku Samariya,

9 Koma panali mneneri wa Yehova pomwepo, dzina lace Odedi; naturuka iye kukomana nayo nkhondo ikudzayo ku Samariya, nanena nao, Taonani, popeza Yehova Mulungu wa makolo anu anakwiya ndi Yuda, anawapereka m'dzanja lanu, nimunawapha ndi kupsa mtima kofikira kumwamba.

10 Ndipo tsopano mukuti mugonjetse ana a Yuda ndi Yerusalemu akhale akapolo ndi adzakazi anu; palibe nanunso kodi mirandu yoparamula kwa Yehova Mulungu wanu?

11 Mundimvere tsono, bwezani andende amene munawatenga ndende a abale anu; pakuti mkwiyo waukali wa Yehova uli pa inu.

12 Pamenepo akuru ena a ana a Efraimu, Azariya mwana wa Yohanana, Berekiya mwana wa Mesilemoti, ndi Yehizikiya mwana wa Salumu, ndi Amasa mwana wa Hadilai, anaukira aja ofuma kunkhondo,

13 nanena nao, Musalowa nao andende kuno; pakuti inu mukuti mutiparamulitse kwa Yehova, kuonjezera pa macimo athu ndi zoparamula zathu; pakuti taparamula kwakukuru, ndipo pali mkwiyo waukali pa Israyeli.

14 Pamenepo eni zida anasiya andende ndi zofunkha pamaso pa akalonga ndi msonkhano wonse.

15 Nanyamuka amuna ochulidwa maina, natenga andende, nabveka ausiwa onse mwa iwo ndi zofunkhazo, nawapatsa zobvala, ndi nsapato, nawadyetsa ndi kuwamwetsa, nawadzoza, nasenza ofoka ao onse pa aburu, nafika nao ku Yeriko, mudzi wa migwalangwa, kwa abale ao; nabwerera iwo kunka ku Samariya.

16 Nthawi yomweyi mfumu Ahazi anatumiza kwa mafumu a Asuri amthandize.

17 Pakuti Aedomu anadzanso, nakantha Yuda, natenga andende.

18 Afilisti omwe adagwa m'midzi ya kucidikha, ndi ya kumwela kwa Yuda, nalanda Betisemesi, ndi Azaloni, ndi Gederoti, ndi Soko ndi miraga yace, ndi Timna ndi miraga yace; nakhala iwo komweko.

19 Pakuti Yehova anacepetsa Yuda cifukwa ca Ahazi mfumu ya Israyeli; popeza iye anacita comasuka pakati pa Yuda, nalakwira Yehova kwambiri.

20 Ndipo Tigilati Pilesere mfumu ya Asuri anadza kwa iye, namsautsa osamlimbikitsa.

21 Pakuti Ahazi analandako za m'nyumba ya Yehova ndi za m'nyumba ya mfumu, ndi ya akalonga, nazipereka kwa mfumu ya Asuri, osathandizidwa nazo.

22 Ndipo nthawi ya nsautso yace anaonjeza kulakwira Yehova, mfumu Ahazi yemweyo.

23 Popeza anaphera nsembe milungu ya Damasiko yomkantha, nati, Popeza milungu ya mafumu a Aramu iwathandiza, ndiiphere nsembe, indithandize inenso. Koma inamkhumudwitsa iye, ndi Aisrayeli onse.

24 Ndipo Ahazi anasonkhanitsa zipangizo za m'nyumba ya Mulungu, naduladula zipangizo za m'nyumba ya Mulungu, natseka pa makomo a nyumba ya Yehova, nadzimangira maguwa a nsembe m'ngondya ziri zonse za Yerusalemu.

25 Ndi m'midzi iri yonse ya Yuda anamanga misanje ya kufukizira milungu yina, nautsa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa makolo ace.

26 Macitidwe ena tsono, ndi njira zace zonse, zoyamba ndi zotsiriza, taonanani, zilembedwa m'buku la mafumu a Yuda ndi Israyeli.

27 Ndi Ahazi anagona ndi makolo ace, namuika m'mudzi wa Yerusalemu; pakuti sanadza naye ku manda a mafumu a Israyeli; ndipo Hezekiya mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

29

1 Hezekiya analowa ufumu wace ali wa zaka makumi awiri mphambu zisanu, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi awiri mphambu zisanu ndi zinai; ndi dzina la mace ndiye Abiya mwana wa Zekariya.

2 Nacita iye zoongoka pamaso pa Yehova, monga umo monse adacitira Davide kholo lace.

3 Caka coyamba ca ufumu wace, mwezi woyamba, anatsegula pa makomo a nyumba ya Yehova, napakonzanso.

4 Nalowetsa ansembe ndi Alevi, nawasonkhanitsa pamalo poyera kum'mawa,

5 nanena nao, Ndimvereni, Alevi inu, dzipatuleni, nimupatule nyumba ya Yehova Mulungu wa makolo anu, ndi kucotsa zoipsa m'malo opatulika.

6 Pakuti analakwa makolo athu, nacita coipa pamaso pa Yehova Mulungu wathu, namsiya, natembenuza nkhope zao osapenya cokhalamo Yehova, namfulatira.

7 Anatsekanso pa khomo la likole, nazima nyalizo, osafukizanso zonunkhira kapena kupereka nsembe zopsereza m'malo opatulika kwa Mulungu wa Israyeli.

8 Motero mkwiyo wa Yehova unali pa Yuda ndi Yerusalemu, nawapereka anjenjemere, nakhale codabwiza ndi cotsonyetsa, monga umo muonera m'maso mwanu.

9 Pakuti taonani, makolo athu adagwa ndi lupanga, ndi ana athu amuna ndi akazi ndi akazi athu ali andende cifukwa ca ici.

10 Tsono mumtima mwanga nditi ndicite cipangano ndi Yehova Mulungu wa Israyeli, kuti mkwiyo wace waukali utembenuke kuticokera.

11 Ana anga, musazengereza tsopano; popeza Yehova anakusankhani inu muime pamaso pace, kumtumikira Iye, ndi kuti mukhale atumiki ace ndi kufukiza zonunkhira.

12 Pamenepo ananyamuka Alevi, Mahati mwana wa Amasai ndi Yoeli mwana wa Azariya, a ana a Akohati; ndi a ana a Merari, Kisi mwana wa Abidi, ndi Azariya mwana wa Yehaleleli; ndi a Agerisoni, Yowa mwana wa Zima, ndi Edeni mwana wa Yowa;

13 ndi a ana a Elizafana, Simri ndi Yeueli; ndi a ana a Asafu, Zekariya ndi Mataniya;

14 ndi a ana a Hemani, Yehudi ndi Simei ndi a ana a Yedutuni, Semaya ndi Uziyeli,

15 Ndipo anamemeza abale ao, nadzipatula, nalowa monga adawauza mfumu mwa mau a Yehova, kuyeretsa nyumba ya Yehova.

16 Ndipo ansembe analowa m'kati mwace mwa nyumba ya Yehova kuiyeretsa, naturutsira ku bwalo la nyumba ya Yehova zoipsa zonse anazipeza m'Kacisi wa Yehova. Nazilandira Alevi, kuziturutsira kunja ku mtsinje wa Kedroni.

17 Anayamba tsono kuipatula tsiku loyamba la mwezi woyamba, nafikira ku likole la Yehova tsiku lacisanu ndi citatu la mwezi, naipatula nyumba ya Yehova m'masiku asanu ndi atatu; natsiriza tsiku lakhumi ndi cisanu ndi cimodzi.

18 Pamenepo analowa m'katimo kwa mfumu Hezekiya, nati, Tayeretsa nyumba yonse ya Yehova, ndi guwa la nsembe yopsereza, ndi zipangizo zace zonse, ndi gome la mkate woonekera, ndi zipangizo zace zonse.

19 Zipangizo zonse zomwe adazitaya mfumu Ahazi m'ufumu wace m'kulakwa kwace kuja, tazikonza, ndi kuzipatula; ndipo taonani, ziri ku guwa la nsembe la Yehova.

20 Pamenepo mfumu Hezekiya analawira mamawa, nasonkhanitsa akalonga a m'mudzi, nakwera kumka ku nyumba ya Yehova.

21 Ndipoanabweranazong'ombe zisanundi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri, ndi atonde asanu ndi awiri, zikhale nsembe yaucimo ya ufumu, ndi ya malo opatulika, ndi ya Yuda. Ndipo anawauza ansembe ana a Aroni azipereke pa guwa la nsembe la Yehova.

22 Momwemo anapha ng'ombezo, ndi ansembe analandira mwazi, nauwaza pa guwa la nsembe, napha nkhosa zamphongozo, nawaza mwazi pa guwa la nsembe; anaphanso ana a nkhosawo, nawaza mwazi pa guwa la nsembe.

23 Pamenepo anayandikiza nao atonde a nsembe yaucimo pamaso pa mfumu ndi msonkhano; ndipo iwo anawasanjika manja ao,

24 ndi ansembewo anawapha, nacita nsembe yaucimo ndi mwazi wao pa guwa la nsembe, kucita cotetezera Aisrayeli onse; pakuti mfumu idauza kuti nsembe yopsereza ndi nsembe yaucimo zikhale za Aisrayeli onse.

25 Ndipo anaika Alevi m'nyumba ya Yehova ndi nsanje, ndi zisakasa, ndi azeze, monga umo adauzira Davide, ndi Gadi mlauli wa mfumu, ndi Natani mneneriyo; pakuti lamulo ili lidafuma kwa Yehova mwa aneneri ace.

26 Alevi tsono anaimirira ndi zoyimbira za Davide, ndi ansembe anakhala ndi malipenga.

27 Nanena Hezekiya kuti apereke nsembe yopsereza pa guwa la nsembe. Ndipo pakuyamba nsembe yopsereza, inayambanso nyimbo ya Yehova ndi malipenga, pamodzi ndi zoyimbira za Davideyo mfumu ya Israyeli.

28 Ndi msonkhano wonse unalambira, ndi oyimbira anayimba, ndi amalipenga anaomba; zonsezi mpaka adatsiriza nsembe yopsereza.

29 Ndipo atatsiriza kuperekaku, mfumu ndi onse opezeka pamodzi naye anawerama, nalambira.

30 Hezekiya mfumu ndi akalonga anauzanso Alevi ayimbire Yehova zomlemekeza ndi mau a Davide ndi a Asafu mlauli. Ndipo anayimbira zomlemekeza mokondwera, nawerama mitu yao, nalambira.

31 Pamenepo Hezekiya anayankha, nati, Tsopano mwadzipatulira kwa Yehova, senderani, bwerani nazo nsembe zophera ndi nsembe zoyamika ku nyumba ya Yehova. Ndi msonkhano unabwera nazo nsembe zophera ndi nsembe zoyamika, ndi onse a mtima wofuna mwini anabwera nazo nsembe zopsereza.

32 Ndi kuwerenga kwace kwa nsembe zopsereza unabwera nazo msonkhanowo ndiko ng'ombe makumi asanu ndi awiri, nkhosa zamphongo zana limodzi, ndi ana a nkhosa mazana awiri; zonsezi nza nsembe yopsereza ya Yehova.

33 Ndi zinthu, zopatulika zinafikira ng'ombe mazana asanu ndi limodzi, ndi nkhosa zikwi zitatu.

34 Koma ansembe anaperewera, osakhoza kusenda nsembe zonse zopsereza; m'mwemo abale ao Alevi anawathandiza, mpaka idatha nchitoyi, mpaka ansembe adadzipatula; pakuti Alevi anaposa ansembe m'kuongoka mtima kwao kudzipatula.

35 Ndiponso zidacuruka nsembe zopsereza, pamodzi ndi mafuta a nsembe zamtendere, ndi nsembe zothira za nsembe yopsereza iri yonse. Momwemo utumiki wa nyumba ya Yehova unalongosoka.

36 Nakondwera Hezekiya ndi anthu onse pa ici Mulungu adakonzeratu; pakuti cinthuci cidacitika modzidzimutsa.

30

1 Ndipo Hezekiya anatumiza kwa Israyeli ndi Yuda onse, nalembanso akalata kwa Efraimu ndi Manase, kuti abwere ku nyumba ya Yehova ku Yerusalemu, kucitira Yehova Mulungu wa Israyeli Paskha.

2 Pakuti mfumu idapangana ndi akuru ace, ndi msonkhano wonse wa m'Yerusalemu, kuti acite Paskha mwezi waciwiri.

3 Pakuti sanakhoza kumcita nthawi ija, popeza ansembe odzipatulira sanafikira, ndi anthu sadasonkhana ku Yerusalemu.

4 Ndipo cinthuci cinayenera m'maso mwa mfumu ndi msonkhano wonse.

5 Motero anakhazikitsa mau kulalikira mwa Israyeli lonse, kuyambira Beereseba kufikira ku Dani, kuti abwere kucitira Yehova Mulungu wa Israyeli Paskha ku Yerusalemu; pakuti nthawi yaikuru sanacita monga mudalembedwa.

6 Tsono amtokoma anamuka ndi akalata ofuma kwa mfumu ndi akuru ace mwa Israyeli ndi Yuda lonse, monga inauza mfumu ndi kuti, Inu ana a Israyeli, bwerani kwa Yehova Mulungu wa Abrahamu, Isake, ndi Israyeli, kuti Iye abwere kwa otsala anu opulumuka m'dzanja la mafumu a Asuri.

7 Ndipo musamakhala ngati makolo anu ndi abale anu, amene anai akwira Yehova Mulungu wa makolo ao, motero kuti anawapereka apasuke, monga mupenya,

8 Musamakhala ouma khosi monga makolo anu; koma gwiranani dzanja ndi Yehova, nimulowe m'malo ace opatulika, amene anapatula kosatha, ndi kutumikira Yehova Mulungu wanu; kuti mkwiyo wace waukali utembenuke kwa inu.

9 Pakuti mukabwera kwa Yehova, abale anu ndi ana anu adzapeza cifundo pamaso pa iwo anawatenga ndende, nadzalowanso m'dziko muno; pakuti Yehova Mulungu wanu ngwa cisomo ndi cifundo; sadzakuyang'anirani kumbali ngati mubwera kwa Iye,

10 Ndipo amtokoma anapitira m'midzi m'midzi mwa dziko la Efraimu ndi Manase, mpaka Zebuloni; koma anawaseka pwepwete nawanyodola.

11 Komatu ena a Aseri ndi Manase ndi a Zebuloni anadzicepetsa, nadza ku Yerusalemu.

12 Ku Yuda komwe kunali dzanja la Mulungu lakuwapatsa mtima umodzi, kucita cowauza mfumu ndi akuru mwa mau a Yehova.

13 Nasonkhana ku Yerusalemu anthu ambiri kucita madyerero a mkate wopanda cotupitsa mwezi waciwiri, msonkhano waukuru ndithu.

14 Ndipo anauka nacotsa maguwa a nsembe okhala m'Yerusalemu, nacotsa pofukizira zonunkhira, naziponya m'mtsinje wa Kedroni.

15 Pamenepo anaphera Paskha tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi waciwiri, ndipo ansembe ndi Alevi anacita manyazi, nadzipatula, nabwera nazo nsembe zopsereza ku nyumba ya Yehova.

16 Naima m'malo mwao mwa kulongosoka kwao, monga mwa cilamulo ca Mose munthu wa Mulunguyo; ansembe anawaza mwazi, ataulandira ku dzanja la Alevi.

17 Pakuti munali ambiri mumsonkhano sanadzipatula; potero Alevi anayang'anira kupha za Paskha kwa ali yense wosakhala woyera, kuwapatulira Yehova.

18 Pakuti, anthu aunyinji, ndiwo ambiri a Efraimu, ndi Manase, Isakara, ndi Zebuloni, sanadziyeretsa, koma anadya Paskha mosati monga munalembedwa.

19 Koma Hezekiya anawapempherera, ndi kuti, Yehova wabwino akhululukire yense wakuika mtima wace kufuna Mulungu Yehova, Mulungu wa makolo ace, cinkana sanayeretsedwa monga mwa mayeretsedwe a malo opatulika.

20 Ndipo Yehova anamvera Hezekiya, nawaciritsa anthu.

21 Ndipo ana a Israyeli opezeka m'Yerusalemu anacita madyerero a mkate wopanda cotupitsa masiku asanu ndi awiri ndi cimwemwe cacikuru; ndi Alevi ndi ansembe analemekeza Yehova tsiku ndi tsiku ndi zoyimbira zakuliritsa kwa Yehova.

22 Ndipo Hezekiya ananena motonthoza mtima kwa Alevi onse akuzindikira bwino za utumiki wa Yehova. Ndipo anadya pamkomano masiku asanu ndi awiri, naphera nsembe zoyamika, ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa makolo ao.

23 Ndipo msonkhano wonse unapangana kucita masiku asanu ndi awiri ena, nacita masiku asanu ndi awiri ena ndi cimwemwe.

24 Pakuti Hezekiya mfumu ya Yuda anapatsa msonkhano ng'ombe cikwi cimodzi, ndi nkhosa zikwi zisanu ndi ziwiri; ndi akuru anapatsa msonkhano ng'ombe cikwi cimodzi, ndi nkhosa zikwi khumi; ndipo ansembeambiri adadzipatula,

25 Ndi msonkhano wonse wa Yuda, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi, ndi msonkhano wonse wocokera kwa Israyeli, ndi alendo ocokera ku dziko la Israyeli, ndi okhala m'Yuda, anakondwera.

26 Momwemo munali cimwemwe cacikuru m'Yerusalemu; pakuti kuyambira masiku a Solomo mwana wa Davide mfumu ya Israyeli simunacitika cotero m'Yerusalemu.

27 Pamenepo ansembe Alevi anauka, nadalitsa anthu; ndi mau ao anamveka, ndi pemphero lao lidakwera pokhala pace popatulika Kumwamba.

31

1 Citatha ici conse tsono, Aisrayeli onse opezekako anaturuka kumka ku midzi ya Yuda, naphwanya zoimiritsa, nalikha zifanizo, nagamula misanje ndi maguwa a nsembe m'Yuda monse, ndi m'Benjamini, m'Efraimunso, ndi m'Manase, mpaka adaziononga zonse. Pamenepo ana onse a Israyeli anabwerera, yense ku dziko lace ndi ku midzi yao.

2 Ndipo Hezekiya anaika zigawo za ansembe ndi Alevi, monga mwa magawidwe ao, yense monga mwa utumiki wace, ndi ansembe ndi Alevi, acite nsembe zopsereza ndi nsembe zoyamika kutumikira, ndi kuyamika, ndi kulemekeza, ku zipata za cigono ca Ambuye.

3 Naikanso gawo la mfumu lotapa pa cuma cace la nsembe zopsereza, ndilo la nsembe zopsereza za m'mawa ndi madzulo, ndi la nsembe zopsereza za masabata, ndi za pokhala mwezi, ndi za nyengo zoikika, monga mulembedwa m'cilamulo ca Yehova.

4 Anauzanso anthu okhala m'Yerusalemu apereke gawo la ansembe ndi Alevi, kuti iwowa alimbike m'cilamulo ca Yehova.

5 Ndipo pobuka mau aja, ana a Israyeli anapereka mocuruka, zobala zoyamba za tirigu, vinyo, ndi mafuta, ndi uci, ndi za zipatso zonse za m'minda, ndi limodzi la magawo khumi la zonse anabwera nazo mocuruka.

6 Ndi ana a Israyeli ndi Yuda okhala m'midzi ya Yuda, iwonso anabwera nalo limodzi la magawo khumi la ng'ombe, ndi nkhosa, ndi limodzi la magawo khumi la zinthu zopatulika, zopatulikira Yehova Mulungu wao; naziunjika miyuru miyuru,

7 Mwezi wacitatu anayamba kuika miyalo ya miyuruyi, naitsiriza mwezi wacisanu ndi ciwiri.

8 Ndipo pamene Hezekiya ndi akuru ace anadza, naona miyuruyi, analemekeza Yehova, nadalitsa anthu ace Aisrayeli.

9 Pamenepo Hezekiya anafunsana ndi ansembe ndi Alevi za miyuruyi,

10 Ndipo Azariya wansembe wamkuru wa nyumba ya Zadoki anamyankha, nati, Ciyambire anthu anabwera nazo zopereka ku nyumba ya Yehova, tadya, takhuta, ndipo zatitsalira zambiri; pakuti Yehova anadalitsa anthu ace; ndipo suku kucuruka kwa cotsala.

11 Pamenepo Hezekiya anawauza akonze zipinda m'nyumba ya Yehova; nazikonza.

12 Ndipo anabwera nazo nsembe zokweza, ndi amodzi a magawo khumi, ndi zinthu zopatulika, mokhulupirika; ndi mkuru woyang'anira izi ndiye Konaniya Mlevi, ndi Simei mng'ono wace ndiye wotsatana naye.

13 Ndi Yeiyeli, ndi Azaziya, ndi Nahati, ndi Asaheli, ndi Yerimoti, ndi Yozabadi, ndi Eliyeli, ndi Ismakiya, ndi Mahati, ndi Benaya, ndiwo akapitao omvera Konaniya ndi Simei mng'ono wace, oikidwa ndi Hezekiya mfumu ndi Azariya mkuru wa ku nyumba ya Mulungu.

14 Ndipo Kore mwana wa Imna Mlevi, wa ku cipata ca kum'mawa, anayang'anira zopereka zaufulu za Mulungu, kugawira nsembe zokweza za Yehova, ndi zopatulikitsa.

15 Ndi omvera iye ndiwo Edeni, ndi Minyamini, ndi Yesuwa; ndi Semaya, Amariya, ndi Sekaniya, m'midzi ya ansembe, kugawira abale ao m'zigawo zao mokhulupirika, akuru monga ang'ono;

16 pamodzi ndi iwo oyesedwa mwa cibadwidwe ca amuna, kuyambira a zaka zitatu ndi mphambu, kwa ali yense amene adalowa m'nyumba ya Yehova, monga mwa nchito yace pa tsiku lace, kukacita za utumiki wao m'udikiro wao monga mwa zigawo zao;

17 ndi iwo oyesedwa mwa cibadwidwe ca ansembe mwa nyumba za makolo ao, ndi Alevi, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu m'udikiro mwao, monga mwa zigawo zao;

18 ndi iwo oyesedwa mwa cibadwidwe ca ana ao ang'ono onse, akazi ao, ndi ana ao amuna ndi akazi, mwa msonkhano wonse; pakuti m'kukhulupirika kwao anadzipatula akhale opatulika;

19 panalinso amuna mwa ana a Aroni ansembe, okhala m'minda ya kubusa kwa midzi yao, m'mudzi uli wonse, ochulidwa maina ao, agawire amuna onse mwa ansembe, ndi onse mwa Alevi, oyesedwa mwa cibadwidwe magawo ao.

20 Momwemo anacita Hezekiya mwa Yuda lonse nacita cokoma, ndi coyenera, ndi cokhulupirika, pamaso pa Yehova Mulungu wace.

21 Ndipo m'nchito iri yonse anaiyamba m'utumiki wa nyumba ya Mulungu, ndi m'cilamulo, ndi m'mauzo, kufuna Mulungu wace, anacita ndi mtima wace wonse, nalemerera nayo.

32

1 Zitatha zinthu izi zokhulupirika, anadza Sanakeribu mfumu ya Asuri, nalowera Yuda, namangira midzi yamalinga misasa, nati adzigonjetsere iyi.

2 Ndipo pakuona Hezekiya kuti wadza Sanakeribu, ndi kuti nkhope yace inalunjikitsa kuyambana nkhondo ndi Yerusalemu,

3 anapangana ndi akuru ace ndi amphamvu ace, kutseka madzi a m'akasupe okhala kunja kwa mudzi; namthandiza iwo.

4 Nasonkhana anthu ambiri, natseka akasupe onse, ndi mtsinje woyenda pakati pa dziko, ndi kuti, Angafike mafumu a Asuri ndi kupeza madzi ambiri.

5 Ndipo analimbika mtima, namangitsa linga lonse mopasuka, nalikweza mpaka pansanja, ndi linga lina kunja kwace, nalimbitsa Milo m'mudzi wa Davide, napanga zida ndi zikopa zocuruka.

6 Naika akazembe a nkhondo alamulire anthu, nawasonkhanitsira kuli iye ku bwalo la ku cipata ca mudzi, nanena nao motonthoza mtima wao ndi kuti,

7 Limbani, mulimbike mtima, musaopa kapena ku tenga nkhawa pankhope pa mfumu ya Asuri ndi aunyinji okhala naye; pakuti okhala nafe acuruka koposa okhala naye;

8 pamodzi ndi iye pali dzanja la thupi lanyama; koma pamodzi ndi ife pali Yehova Mulungu wathu, kutithandiza ndi kutigwirira nkhondo. Ndipo anthu anacirikizika ndi mau a Hezekiya mfumu ya Yuda.

9 Pambuyo pace Sanakeribu mfumu ya Asuri, akali ku Lakisi ndi mphamvu yace yonse pamodzi naye, anatuma anyamata kwa Hezekiya mfumu ya Yuda, ndi kwa Ayuda onse okhala ku Yerusalemu, ndi kuti,

10 Atero Sanakeribu mfumu ya Asuri, Mutama ciani kuti mukhala m'linga m'Yerusalemu?

11 Sakukopani Hezekiya, kuti akuperekeni mufe nayo njala ndi ludzu, ndi kuti, Yehova Mulungu wathu adzatilanditsa m'dzanja la mfumu ya Asuri?

12 Sanaicotsa misanje yace ndi maguwa ace a nsembe Hezekiya yemweyo, nauza Yuda ndi Yerusalemu, ndi kuti, Mugwadire ku guwa la nsembe limodzi ndi kufukiza zonunkhira pamenepo?

13 Simudziwa kodi comwe ine ndi makolo anga tacitira anthu onse a m'maikomo? Kodi milungu ya mitundu ya anthu inakhoza konse kulanditsa dziko lao m'dzanja langa?

14 Ndi uti mwa milungu yonse ya mitunduyi ya anthu, amene makolo anga anawaononga konse, unakhoza kulanditsa anthu ace m'dzanja mwanga, kuti Mulungu wako adzakhoza kukulanditsa iwe m'dzanja mwanga?

15 Ndipo tsono, asakunyengeni Hezekiya, ndi kukukopani motero, musamkhulupirira; pakuti palibe mulungu wa mtundu uli wonse wa anthu, kapena ufumu uli wonse, unakhoza kulanditsa anthu ace m'dzanja mwanga; ndipo kodi Mulungu wanu adzakulanditsani inu m'dzanja langa?

16 Ndipo anyamata ace anaonjeza kunena motsutsana ndi Yehova Mulungu, ndi mnyamata wace Hezekiya,

17 Analemberanso akalata a kunyoza Yehova Mulungu wa Israyeli, ndi kunena motsutsana ndi Iye, ndi kuti, Monga milungu ya mitundu ya anthu a m'maiko, imene siinalanditsa anthu ao m'dzanja langa, momwemo Mulungu wa Hezekiya sadzalanditsa anthu ace m'dzanja mwanga.

18 Ndipo anapfuula ndi mau akuru m'cinenedwe ca Ayuda kwa anthu a m'Yerusalemu okhala palinga, kuwaopsa ndi kuwabvuta, kuti alande mudziwu.

19 Nanenera Mulungu wa Yerusalemu, monga umo amanenera milungu ya mitundu ya anthu a pa dziko lapansi, ndiyo nchito ya manja a anthu.

20 Ndipo Hezekiya mfumu, ndi Yesaya mneneri mwana wa Amozi, anapemphera pa ici, napfuulira Kumwamba.

21 Ndipo Yehova anatuma wamthenga amene anaononga ngwazi zamphamvu zonse, ndi atsogoleri, ndi akazembe, ku cigono ca mfumu ya Asuri. Nabwerera iye ndi nkhope yamanyazi ku dziko lace. Ndipo atalowa m'nyumba ya mulungu wace, iwo oturuka m'matumbo mwace anamupha ndi lupanga pomwepo.

22 Momwemo Yehova analanditsa Hezekiya ndi okhala m'Yerusalemu m'dzanja la Sanakeribu mfumu ya Asuri, ndi m'dzanja la onse ena, nawatsogolera monsemo.

23 Ndipo ambiri anabwera nayo mitulo kwa Yehova ku Yerusalemu, ndi za mtengo wace, kwa Hezekiya mfumu ya Yuda; nakwezeka iye pamaso pa amitundu onse kuyambira pomwepo.

24 Masiku omwe aja Hezekiya anadwala pafupi imfa; ndipo anapemphera kwa Yehova; ndi Iye ananena naye, nampatsa cizindikilo codabwiza.

25 Koma Hezekiya sanabwezera monga mwa cokoma anamcitira, pakuti mtima wace unakwezeka; cifukwa cace unamdzera mkwiyo iye, ndi Yuda, ndi Yerusalemu.

26 Koma Hezekiya anadzicepetsa m'kudzikuza kwa mtima wace, iye ndi okhala m'Yerusalemu, momwemo mkwiyo wa Yehova sunawadzera masiku a Hezekiya.

27 Ndipo cuma ndi ulemu zinacurukira Hezekiya, nadzimangira iye zosungiramo siliva, ndi golidi, ndi timiyala ta mtengo wace, ndi zonunkhira, ndi zikopa, ndi zipangizo zokoma ziri zonse;

28 ndi nyumba zosungiramo zipatso za tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta, ndi zipinda za nyama iri yonse, ndi makola a zoweta.

29 Nadzimangiranso midzi, nadzionera nkhosa ndi ng'ombe zocuruka; pakuti Mulungu adampatsa cuma cambirimbiri.

30 Hezekiya yemweyo anatseka kasupe wa kumtunda wa madzi a Gihoni, nawapambutsa atsikire ku madzulo kwa mudzi wa Davide. Ndipo Hezekiya analemerera nazo nchito zace zonse.

31 Koma pokhala naye akazembe a akalonga a ku Babulo, amene anatumiza kwa iye kufunsira za codabwiza cija cidacitika m'dzikomo, Mulungu anamsiya, kumuyesa, kuti adziwe zonse za mumtima mwace.

32 Macitidwe ena tsono a Hezekiya, ndi nchito zace zokoma, taonani, zilembedwa m'masomphenya a Yesaya mneneri mwana wa Amozi, ndi m'buku la mafumu a Yuda ndi Israyeli.

33 Ndipo Hezekiya anagona ndi makolo ace, namuika polowerera ku manda a ana a Davide; ndi Ayuda onse ndi okhala m'Yerusalemu anamcitira ulemu pa imfa yace. Ndipo Manase mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

33

1 Manase anali wa zaka khumi ndi ziwiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi asanu mphambu zisanu.

2 Nacita coipa pamaso pa Yehova, monga mwa zonyansa za amitundu, amene Yehova anawacotsa m'dziko mwao pamaso pa ana a Israyeli.

3 Pakuti anamanganso misanje adaipasula Hezekiya atate wace, nautsira Abaala maguwa a nsembe, napanga zifanizo, nalambira khamu lonse la kuthambo, nalitumikira.

4 Namanga maguwa a nsembe m'nyumba ya Yehova, imene Yehova adati, M'Yerusalemu mudzakhala dzina langa ku nthawi zonse.

5 Namangiranso khamu lonse la kuthambo maguwa a nsembe m'mabwalo awiri a nyumba ya Yehoya.

6 Anapititsanso ana ace pamoto m'cigwa ca ana a Hinomu, naombeza maula, nasamalira malodza, nacita zanyanga, naika obwebweta ndi openduza; anacita zoipa zambiri pamaso pa Yehova kuutsa mkwiyo wace.

7 Ndipo anaika cifanizo cosema ca fanolo adacipanga m'nyumba ya Mulungu, imene Mulungu adati kwa Davide ndi Solomo mwana wace, M'nyumba muno ndi m'Yerusalemu umene ndausankha m'mafuko onse a Israyeli ndidzaika dzina langa ku nthawi zonse;

8 ndipo sindidzasunthanso phazi la Israyeli ku dziko ndaliikira makolo anu; pokhapo asamalire kucita zonse ndawalamulira, cilamulo conse, ndi malemba, ndi maweruzo, mwa dzanja la Mose.

9 Koma Manase analakwitsa Yuda ndi okhala m'Yerusalemu, kotero kuti anacita coipa koposa amitundu, amene Yehova anawaononga pamaso pa ana a Israyeli.

10 Ndipo Yehova analankhula ndi Manase ndi anthu ace, koma sanasamalira.

11 Motero Yehova anawafikitsira akazembe a khamu la nkhondo la mfumu ya Asuri, namgwira Manase ndi zokowera, nammanga matangadza, namuka naye ku Babulo.

12 Ndipo popsinjika iye anapembedza Yehova Mulungu wace, nadzicepetsa kwambiri pamaso pa Mulungu wa makolo ace.

13 Anampempha, ndipo anapembedzeka, namvera kupembedza kwace, nambwezera ku Yerusalemu m'ufumu wace. Pamenepo anadziwa Manase kuti Yehova ndiye Mulungu.

14 Citatha ici tsono iye anaumangira mudzi wa Davide linga lakunja, kumadzulo kwa Gihoni, m'cigwa, mpaka polowera pa cipata cansomba; nazinga Ofeli, nalikweza kwambiri; anaikanso akazembe a nkhondo m'midzi yonse yamalinga ya m'Yuda.

15 Ndipo anacotsa milungu yacilendo, ndi fanoli m'nyumba ya Yehova, ndi maguwa onse a nsembe anawamanga m'phiri la nyumba ya Yehova ndi m'Yerusalemu, nawataya kunja kwa mudzi.

16 Namanga guwa la nsembe la Yehova, napherapo nsembe zamtendere ndi zoyamika, nalamulira Yuda atumikire Yehova Mulungu wa Israyeli.

17 Koma anthu anapherabe nsembe pamisanje; koma anaziphera Yehova Mulungu wao.

18 Macitidwe ena tsono a Manase, ndi pemphero lace kwa Mulungu wace, ndi mau a alauli akunena naye m'dzina la Yehova Mulungu wa Israyeli, taonani, zalembedwa m'niacitidwe a mafumu a Israyeli.

19 Pemphero lace lomwe, ndi m'mene Mulungu anapembedzeka naye, ndi chimo lace lonse, ndi kulakwa kwace, ndi apo anamanga misanje, naimika zifanizo ndi mafano osema asanadzicepetse, taonani, zalembedwa m'buku la mau a Hozai.

20 Momwemo Manase anagona ndi makolo ace, namuika m'nyumba mwace mwace; ndi Amoni mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

21 Amoni ndiye wa zaka makumi awiri mphambu ziwiri polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka ziwiri.

22 Ndipo anacita coipa pamaso pa Yehova, monga umo anacitira Manase atate wace; pakuti Amoni anaphera nsembe mafano osema onse amene adawapanga Manase atate wace, nawatumikira.

23 Koma sanadzicepetsa pamaso pa Yehova, monga umo anadzicepetsera Manase atate wace; koma Amoni amene anacurukitsa kuparamula kwace.

24 Ndipo anyamata ace anampangira ciwembu, namupha m'nyumba yace yace.

25 Koma anthu a m'dziko anapha onse adampangira ciwembu mfumu Amoni; ndi anthu a m'dziko analonga Yosiya mwana wace akhale mfumu m'malo mwace.

34

1 Yosiya ndiye wa zaka zisanu ndi zitatu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi atatu mphambu cimodzi.

2 Nacita zoongoka pamaso pa Yehova, nayenda m'njira za Davide kholo lace, osapambuka ku dzanja lamanja kapena kulamanzere.

3 Pakuti atakhala mfumu zaka zisanu ndi ziwiri akali mnyamata, anayamba kufuna Mulungu wa Davide kholo lace; ndipo atakhala zaka khumi ndi cimodzi anayamba kuyeretsa Yuda ndi Yerusalemu, kuzicotsa misanje, ndi zifanizo, ndi mafano osema, ndi mafano oyenga,

4 Ndipo anthu anagumula maguwa a nsembe a Abaala pamaso pace; nawalikha mafano a dzuwa anakwezeka pamwamba pao; naphwanya zifanizo, ndi mafano osema, ndi mafano oyenga; nazipera, naziwaza pamanda pa iwo amene adaziphera nsembe.

5 Napsereza mafupa a ansembe pa maguwa a: nsembe ao, nayeretsa Yuda ndi Yerusalemu.

6 Nateronso m'midzi ya Manase, ndi Efraimu, ndi Simeoni, mpaka Nafitali, m'mabwinja mwao mozungulira.

7 Nagumula maguwa a nsembe, naperapera zifanizo ndi mafano osema, nalikha mafano a dzuwa onse m'dziko lonse la Israyeli, nabwerera kumka ku Yerusalemu.

8 Atakhala mfumu tsono zaka khumi mphambu zisanu ndi ziwiri, atayeretsa dziko ndi nyumbayi, anatuma safana mwana wa Azaliya, ndi Maseya kazembe wa mudzi, ndi Yona mwana wa Yoadazi wolemba mbiri, akonze nyumba ya Yehova Mulungu wace.

9 Ndipo anadza kwa Hilikiya wansembe wamkulu, napereka ndarama adabwera nazo ku nyumba ya Mulungu, zimene Alevi osunga pakhomo adasonkhanitsa kuzilandira ku dzanja la Manase ndi Efraimu, ndi kwa otsala onse a Israyeli, ndi kwa Yuda yense, ndi Benjamini, ndi kwa okhala m'Yerusalemu.

10 Ndipo anazipereka m'dzanja la anchito oikidwa ayang'anire nyumba ya Yehova; ndi iwo anazipereka kwa anchito akucita m'nyumba ya Yehova, kukonza ndi kulimbitsa nyumbayi;

11 anazipereka kwa amisiri a mitengo ndi omanga nyumba, agule miyala yosema, ndi mitengo ya mitanda yam'mwamba ndi yammunsi ya nyumbazi, adaziononga mafumu a Yuda.

12 Ndipo amunawo anacita nchitoyi mokhulupirika; ndi oikidwa awayang'anire ndiwo Yohati ndi Obadiya, Alevi, a ana a Merari; ndi Zekariya ndi Mesulamu, a ana a Akohati, kuifulumiza; ndi Alevi ena ali yense wa luso la zoyimbira,

13 Anayang'aniranso osenza akatundu, nafulumiza onse akugwira nchito ya utumiki uli wonse; ndi mwa Alevi munali alembi, ndi akapitao, ndi odikira.

14 Ndipo pakuturutsa ndarama zimene adalowa nazo ku nyumba ya Yehova, Hilikiya wansembe anapeza buku la cilamulo la Yehova mwa dzanja la Mose.

15 Ndipo Hilikiya anayankha nati kwa Safani mlembi, Ndapeza buku la cilamulo m'nyumba ya Yehova. Hilikiya napereka buku kwa Safani.

16 Ndi Safani anamuka nalo buku kwa mfumu, nabwezeranso mau kwa mfumu, ndi kuti, Zonse mudazipereka kwa anyamata anu alikuzicita.

17 Nakhuthula ndarama zinapezeka m'nyumba ya Yehova, nazipereka m'manja a akapitao ndi m'manja a anchito.

18 Ndipo Safani mlembi anauza mfumu, ndi kuti, Hilikiya wansembe anandipatsa buku. Nawerengamo Safani pamaso pa mfumu.

19 Ndipo kunali, atamva mfumu mau a cilamulo, anang'amba zobvala zace.

20 Mfumu niuza Hilikiya, ndi Ahikamu mwana wa Safani, ndi Abidoni mwana wa Mikaya, ndi Safani mlembi, ndi Asaya mnyamata wa mfumu, ndi kuti,

21 Mukani, mundifunsire kwa Yehova, ine ndi otsala m'Israyeli ndi Yuda, za mau a m'buku lopezekalo; pakuti ukali wa Yehova atitsanulirawu ndi waukuru; popeza makolo athu sanasunga mau a Yehova kucita monga mwa zonse zolembedwa m'bukumu.

22 Namuka Hilikiya ndi iwo aja adawauza mfumu kwa Hulida mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tokati, mwana wa Hasire wosunga zobvala, amene anakhala m'Yerusalemu m'dera laciwiri, nanena naye mwakuti.

23 Ndipo iye ananena nao, Atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Muuze munthuyo anakutumizani kwa ine,

24 Atero Yehova, Taonani, ndifikitsira malo ano ndi anthu okhala m'mwemo coipa, ndico matemberero onse olembedwa m'buku adaliwerenga pamaso pa mfumu ya Yuda;

25 cifukwa anandisiya Ine, nafukizira milungu yina, kuti autse mkwiyo wanga ndi nchito zonse za manja ao; cifukwa cace ukali wanga utsanulidwa pamalo pano wosazimika.

26 Koma kwa mfumu ya Yuda amene anakutumizani kufunsira kwa Yehova, muzitero kwa iye, Atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Kunena za mau udawamva,

27 popeza mtima wako unali woolowa, ndipo wadzicepetsa pamaso pa Mulungu, pakumva mau ace otsutsana nao malo ano, ndi okhala m'mwemo, ndi kudzicepetsa pamaso panga, ndi kung'amba zobvala zako, ndi kulira pamaso panga; Inenso ndakumvera, ati Yehova.

28 Taona, ndidzakusonkhanitsa ku makolo ako, nudzaikidwa kumanda kwako mumtendere, ndi maso ako sadzapenya zoipa zonse ndidzafikitsira malo ano ndi okhala m'mwemo. Ndipo anambwezera mfumu mau.

29 Pamenepo mfumu inatumiza anthu, nisonkhanitsa akulu akulu onse a Yuda ndi Yerusalemu.

30 Nikwera mfumu ku nyumba ya Yehova ndi amuna onse a m'Yuda, ndi okhala m'Yerusalemu, ndi ansembe ndi Alevi, ndi anthu onse akuru ndi ang'ono; nawerenga iye m'makutu mwao mau onse a buku la cipangano adalipeza m'nyumba ya Yehova.

31 Ndipo mfumu inaimirira pokhala pace, nicita pangano pamaso pa Yehova, kuti adzayenda cotsata Yehova, ndi kusunga malamulo ace, ndi mboni zace, ndi malemba ace, ndi mtima wace wonse, ndi moyo wace wonse, kucita mau a cipangano olembedwa m'bukumu.

32 Naimiritsapo onse okhala m'Yerusalemu ndi m'Benjamini. Ndipo okhala m'Yerusalemu anacita monga mwa cipangano ca Mulungu, Mulungu wa makolo ao.

33 Yosiya nacotsa zonyansa zonse m'maiko onse okhala a ana a Israyeli, natumikiritsa onse opezeka m'lsrayeli, inde kutumikira Yehova Mulungu wao. Masiku ace onse iwo sanapambuka kusamtsata Yehova Mulungu wa makolo ao.

35

1 Pamenepo Yosiya anacitira Yehova Paskha m'Yerusalemu, naphera Paskha tsiku lakhumi ndi cinai la mwezi woyamba.

2 Ndipo anaika ansembe pa udikiro wao, nawalimbikitsa acite utumiki wa nyumba ya Yehova.

3 Nati kwa Alevi akuphunzitsa Aisrayeli onse, ndiwo opatulima Yehova, Ikani likasa lopatulika m'nyumba imene Solomo mwana wa Davide mfumu ya Israyeli anaimanga; silikhalanso katundu pa mapewa anu; tsopano mutumikire Yehova Mulungu wanu, ndi anthu ace Israyeli.

4 Ndipo mudzikonzere monga mwa nyumba za makolo anu, m'zigawo zanu, monga umo adalembera Davide mfumu ya Israyeli, ndi umo adalembera Solomo mwana wace.

5 Ndipo muimirire m'malo opatulika, monga mwa magawidwe a nyumba za makolo za abale anu ana a anthu, akhale nalo onse gawo la nyumba ya makolo ya Alevi.

6 Ndipo muphere Paskha, nimudzipatule ndi kukonzera abale anu, kucita monga mwa mau a Yehova ndi dzanja la Mose.

7 Ndipo Yosiya anapatsa ana a anthu zoweta, ana a nkhosa ndi a mbuzi zikhale zonsezo za nsembe za Paskha kwa ali yense anali komweko; zinafikira zikwi makumi atatu, ndi ng'ombe zikwi zitatu, ndizo zotapa pa cuma ca mfumu.

8 Ndi akulu ace anapatsa nsembe yaufulu kwa anthu, kwa ansembe, ndi kwa Alevi. Hilikiya ndi Zekariya ndi Yehieli, atsogoleri a m'nyumba ya Mulungu, anapatsa ansembe zoweta zazing'ono zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi limodzi, ndi ng'ombe mazana atatu, zikhale nsembe za Paskha.

9 Konaniyanso, ndi Semaya, ndi Netaneli, abale ace, ndi Hasabiya, ndi Yeyeli, ndi Yosabadi, akuru a Alevi, ana patsa Alevi zoweta zazing'ono zikwi zisanu, ndi ng'ombe mazana asanu, zikhale nsembe za Paskha.

10 Momwemo anakonzera kutumikiraku, naima ansembe pokhala pao, ndi Alevi m'zigawo zao, monga umo adawauzira mfumu.

11 Pamenepo anaphera Paskha; ndi ansembe anawaza mwazi adaulandira m'manja mwa Alevi amene anasenda nsembezo.

12 Ndipo anacotsapo nsembe zopsereza, kuti azipereke kwa ana a anthu monga mwa magawidwe a nyumba za makolo; azipereke kwa Yehova monga mulembedwa m'buku la Mose. Natero momwemo ndi ng'ombezo.

13 Ndipo anaoca Paskha pamoto, monga mwa ciweruzo; koma zopatulikazo anaziphika m'miphika, ndi m'mitsuko, ndi m'ziwaya; nazipereka msanga kwa ana onse a anthu.

14 Ndi pambuyo pace anadzikonzera okha ndi ansembe; popeza ansembe, ana a Aroni, analikupereka nsembe zopsereza ndi mafuta mpaka usiku; cifukwa cace Alevi anadzikonzera okha ndi ansembe ana a Aroni.

15 Ndi oyimbira, ana a Asafu, anali pokhala pao, monga adalamulira Davide, ndi Asafu, ndi Hemani, ndi Yedutuni mlauli wa mfumu; ndi olindirira anali pa zipata zonse, analibe kuleka utumiki wao; pakuti abale ao Alevi anawakonzera

16 Momwemo kutumikira konse kwa Yehova kunakonzeka tsiku lomwelo, kucita Paskha, ndi kupereka nsembe zopsereza pa guwa la nsembe la Yehova, monga analamulira mfumu Yosiya.

17 Ndipo ana a Israyeli okhalako anacita Paskha nthawi yomweyo, ndi madyerero a mkate wopanda cotupitsa masiku asanu ndi awiri.

18 Panalibe Paskha wocitika m'Israyeli wonga ameneyu, kuyambira masiku a Samueli mneneri; panalibenso wina wa mafumu a Israyeli anacita Paskha wotere, ngati ameneyu anacita Yosiya, ndi ansembe, ndi Alevi, ndi Ayuda onse, ndi Aisrayeli opezekako, ndi okhala m'Yerusalemu.

19 Yosiya atakhala mfumu zaka khumi ndi zisanu ndi ziwiri anacita Paskha amene.

20 Citatha ici conse, Yosiya atakonza nyumbayi, Neko mfumu ya Aigupto anakwera kuyambana ku Karikemisi ku Firate; ndipo Yosiya anamturukira kuyambana naye.

21 Koma Neko anatuma mithenga kwa iye, ndi kuti, Ndiri ndi ciani ndi inu, mfumu ya Yuda? sindinafika kuyambana ndi inu lero, koma ndi nyumba imene ndiri nayo nkhondo; ndipo Mulungu anati ndifulumire; lekani kubvutana ndi Mulungu amene ali nane, Iye angakuonongeni.

22 Koma Yosiya sanatembenuka nkhope yace kumleka, koma anadzizimbaitsa kuti ayambane naye, osamvera mau a Neko ocokera m'kamwa mwa Mulungu; nadza kuyambana naye m'cigwa ca Megido.

23 Ndipo oponya anayang'anitsa mibvi pa mfumu Yosiya, niti mfumu kwa anyamata ace, Ndicotseni ndalasidwa ndithu.

24 Pamenepo anyamata ace anamturutsa m'gareta, namuika m'gareta waciwiri anali naye, nabwerera naye ku Yerusalemu; nafa iye naikidwa m'manda a makolo ace. Ayuda onse ndi Yerusalemu nalira Yosiya.

25 Ndipo Yeremiya anamlembera Yosiya nyimbo yomlira; ndi oyimbira onse, amuna ndi akazi, amanena za Yosiya nyimbo za maliro zao mpaka lero lino; naziika zikhale lemba m'Israyeli; taonani, zilembedwa m'Nyimbo za Maliro.

26 Macitidwe ena tsono a Yosiya, ndi nchito zace zokoma, monga mulembedwa m'cilamulo ca Yehova,

27 ndi zocita iye, zoyamba ndi zotsiriza, taonani, zilembedwa m'buku la mafumu a Israyeli ndi Yuda.

36

1 Pamenepo anthu a m'dziko anatenga Yehoahazi mwana wa Yosiya, namlonga ufumu m'Yerusalemu, m'malo mwa atate wace.

2 Yehoahazi anali wa zaka makumi awiri mphambu zitatu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu miyezi itatu.

3 Ndipo mfumu ya Aigupto anamcotsera ufumu wace m'Yerusalemu, nasonkhetsa dziko matalente zana limodzi a siliva, ndi talente limodzi la golidi.

4 Ndi mfumu ya Aigupto anamlonga Eliyakimu mng'ono wace mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu, nasintha dzina lace likhale Yehoyakimu. Koma Neko anatenga Yehoahazi mkuru wace, namuka naye ku Aigupto.

5 Yehoyakimu anali wa zaka makumi awiri mphambu zisanu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka khumi ndi cimodzi, nacita coipa pamaso pa Yehova Mulungu wace.

6 Nebukadinezara mfumu ya ku Babulo anakwera kuyambana naye, nammanga ndi matangadza kumuka naye ku Babulo.

7 Nebukadinezara anatenganso zipangizo za nyumba ya Yehova kumka nazo ku Babulo, naziika m'kacisi wace ku Babulo.

8 Macitidwe ena tsono a Yehoyakimu, ndi zonyansa zace anazicita, ndi zija zidapezeka zomtsutsa; taonani, zilembedwa m'buku la mafumu a Israyeli ndi Yuda; ndi Yehoyakini mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

9 Yehoyakini anali wa zaka zisanu ndi zitatu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu miyezi itatu, ndi masiku khumi; nacita coipa pamaso pa Yehova.

10 Ndipo pofikanso nyengo, mfumu Nebukadinezara anatumiza anthu abwere naye ku Babulo, pamodzi ndi zipangizo zokoma za nyumba ya Yehova; nalonga Zedekiya mbale wace mfumu ya Yuda ndi Yerusalemu.

11 Zedekiya anali wa zaka makumi awiri mphambu cimodzi polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka khumi ndi cimodzi,

12 nacita coipa pamaso pa Yehova Mulungu wace; sanadzicepetsa kwa Yeremiya mneneri wakunena zocokera pakamwa pa Yehova.

13 Ndiponso anapandukana naye mfumu Nebukadinezara, amene adamlumbiritsa pa Mulungu; koma anaumitsa khosi lace, nalimbitsa mtima wace kusatembenukira kwa Yehova Mulungu wa Israyeli,

14 Ndiponso ansembe akulu onse ndi anthu anacurukitsa zolakwa zao, monga mwa zonyansa zonse za amitundu, nadetsa nyumba ya Yehova, imene ana patula m'Yerusalemu.

15 Ndipo Yehova Mulungu wa makolo ao anatumiza kwa iwo, ndi dzanja la mithenga yace, nalawirira mamawa kuituma, cifukwa anamvera cifundo anthu ace, ndi pokhala pace;

16 koma ananyodola mithenga ya Mulungu, napeputsa mau ace, naseka aneneri ace, mpaka ukali wa Mulungu unaukira anthu ace, mpaka panalibe colanditsa.

17 Pakuti Iye anawakweretsera mfumu ya Akasidi, ndiye anawaphera anyamata ao ndi lupanga, m'nyumba ya malo ao opatulika, osacitira cifundo mnyamata kapena namwali, mkulu kapena nkhalamba; Mulungu anawapereka onse m'dzanja lace.

18 Ndi zipangizo zonse za nyumba ya Mulungu, zazikuru ndi zazing'ono, ndi cuma ca nyumba ya Yehova, ndi cuma ca mfumu, ndi ca akalonga ace, anabwera nazo zonsezi ku Babulo.

19 Ndipo anatentha nyumba ya Mulungu, nagumula linga la Yerusalemu, natentha nyumba zace zonse zacifumu ndi moto, naononga zipangizo zace zonse zokoma.

20 Ndi iwo amene adapulumuka kulupanga anamuka nao ku Babulo, nakhala iwo anyamata ace, ndi a ana ace, mpaka mfumu ya Perisiya idacita ufumu;

21 kuti akwaniridwe mau a Yehova pakamwa pa Yeremiya, mpaka dziko linakondwera nao masabata ace; masiku onse a kupasuka kwace linasunga sabata, kukwaniritsa zaka makumi asanu ndi awiri.

22 Caka coyamba tsono ca Koresi mfumu ya Perisiya, kuti akwaniridwe mau a Yehova pakamwa pa Yeremiya, Yehova anautsa mzimu wa Koresi mfumu ya Perisiya, kuti abukitse mau m'ufumu wace wonse, nawalembenso, ndi kuti,

23 Atero Koresi mfumu ya Perisiya, Yehova Mulungu Wam'mwamba anandipatsa maufumu onse a pa dziko lapansi, nandilangiza ndimmangire nyumba m'Yerusalemu, ndiwo ku Yuda. Ali yense mwa inu a anthu ace onse, Yehova Mulungu wace akhale naye, akwereko.