1

1 MASOMPHENYA a Yesaya mwana wa Amozi, amene iye anaona, onena za Yuda ndi Yerusalemu, masiku a Uziya, Yotamu, Ahazi, ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.

2 Imvani, miyamba inu, chera makutu, iwe dziko lapansi, cifukwa Yehova wanena, Ndakulitsa ndipo ndalera ana, ndipo iwo anandipandukira Ine.

3 Ng'ombe idziwa mwini wace, ndi buru adziwa pomtsekereza: koma Israyeli sadziwa, anthu anga sazindikira.

4 Mtundu wocimwa inu, anthu olemedwa ndi mphulupulu, mbeu yakucita zoipa, ana amene acita moononga, iwo amsiya Yehova, iwo amnyoza Woyera wa Israyeli, iwo adana naye nabwerera m'mbuyo.

5 Nanga bwanji mukali cimenyedwere kuti inu mulikupandukirabe? Mutu wonse ulikudwala, ndi mtima wonse walefuka.

6 Kucokera pansi pa phazi kufikira kumutu m'menemo mulibe cangwiro; koma mabala, ndi mikwingwirima, ndi zironda; sizinapole, ngakhale kumangidwa, ngakhale kupakidwa mafuta.

7 Dziko lanu liri bwinja; midzi yanu yatenthedwa ndi moto; dziko lanu alendo alimkudya pamaso panu; ndipo liri labwinja monga lagubuduzidwa ndi alendo.

8 Ndipo mwana wamkazi wa Ziyoni wasiyidwa ngati citando ca m'munda wamphesa, ngati cilindo ca m'munda wamankhaka, ngati mudzi wozingidwa ndi nkhondo.

9 Akadapanda Yehova wa makamu kutisiyira otsala ang'onong'ono ndithu, ife tikanakhala ngati Sodomu, ife tikadanga Gomora.

10 Imvani mau a Yehova inu olamulira a Sodomu, cherani makutu ku cilamulo ca Mulungu wathu, inu anthu a Gomora.

11 Nditani nazo nsembe zanu zocurukazo? ati Yehova; ndakhuta nazo nsembe zopsereza za nkhosa zamphongo ndi mafuta a nyama zonenepa; sindisekera ndi mwazi wa ng'ombe zamphongo, ngakhale wa ana a nkhosa, ngakhale wa atonde.

12 Pakudzaonekera inu pamaso pa Ine, ndani wafuna cimeneci m'dzanja lanu, kupondaponda m'mabwalo mwanga?

13 Musadze nazonso, nsembe zacabecabe; nsembe zofukiza zindinyansa; tsiku lokhala mwezi ndi sabata, kumema masonkhano, sindingalole mphulupulu ndi masonkhano.

14 Masiku anu okhala mwezi ndi nthawi za mapwando anu mtima wanga uzida; zindibvuta Ine; ndalema ndi kupirira nazo.

15 Ndipo pamene mutambasula manja anu, ndidzakubisirani inu maso anga; inde pocurukitsa mapemphero anu Ine sindidzamva; manja anu adzala mwazi.

16 Sambani, dziyeretseni; cotsani macitidwe anu oipa pamaso panga; lekani kucita zoipa;

17 phunzirani kucita zabwino; funani ciweruzo; thandizani osautsidwa, weruzirani ana amasiye, munenere akazi amasiye.

18 Tiyeni, tsono, tiweruzane, ati Yehova; ngakhale zoipa zanu ziri zofiira, zidzayera ngati matalala; ngakhale ziri zofiira ngati kapezi, zidzakhala ngati ubweya wa nkhosa, woti mbu.

19 Ngati inu muli ofuna ndi omvera, mudzadya zabwino za dziko,

20 koma ngati mukana ndi kupanduka, mudzathedwa ndi lupanga; cifukwa m'kamwa mwa Yehova mwatero.

21 Mudzi wokhulupirika wasanduka wadama! wodzala ciweruzowo! cilungamo cinakhalamo koma tsopano ambanda.

22 Siliva wako wasanduka mphala, vinyo wako wasanganizidwa ndi madzi.

23 Akuru ako apanduka, ali anzao a mbala; onse akonda mitulo, natsata zokometsera mirandu; iwo saweruzira amasiye; ngakhale mlandu wa mkazi wamasiye suwafika.

24 Cifukwa cace Yehova ati, Yehova wa makamu wamphamvu wa Israyeli, Ha! ndidzatonthoza mtima wanga pocotsa ondibvuta, ndi kubwezera cilango adani anga;

25 ndipo ndidzaikanso dzanja langa pa iwe, ndi kukusungunula kukusiyanitsa iwe ndi mphala yako, ndipo ndidzacotsa seta wako wonse:

26 ndidzabweza oweruza ako monga poyamba, ndi aphungu ako monga paciyambi; pambuyo pace udzachedwa Mudzi wolungama, mudzi wokhulupirika.

27 Ziyoni adzaomboledwa ndi ciweruzo, ndi otembenuka mtima ace ndi cilungamo.

28 Koma kupasula kwa olakwa ndi kwa ocimwa kudzakhala kumodzi, ndi iwo amene asiya Yehova adzathedwa.

29 Cifukwa adzakhala ndi manyazi, cifukwa ca mitengo yathundu munaikhumba, ndipo inu mudzagwa nkhope, cifukwa ca minda imene mwaisankha.

30 Cifukwa mudzakhala ngati mtengo wathundu, umene tsamba lace linyala, ngatinso munda wopanda madzi.

31 Ndimo wamphamvu adzakhala ngati cingwe cabwazi, ndi nchito yace ngati nthethe; ndipo zonse zidzayaka moto pamodzi, opanda wozimitsa.

2

1 Mau amene Yesaya mwana wa Amozi anaona, onena za Yuda ndi Yerusalemu.

2 Ndipo padzakhala masiku otsiriza, kuti phiri la nyumba ya Yehova lidzakhazikika pa nsonga ya mapiri, ndipo lidzakwezedwa pamwamba pa zitunda; mitundu yonse idzasonkhana kumeneko.

3 Ndipo anthu ambiri adzanka, nati, Tiyeni tikwere kunka ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo; ndipo Iye adzatiphunzitsa za njira zace, ndipo tidzayenda m'mayendedwe ace; cifukwa m'Ziyoni mudzaturuka cilamulo, ndi mau a Yehova kucokera m'Yerusalemu.

4 Iye adzaweruza pakati pa akunja, adzadzudzula mitundu yambiri ya anthu; ndipo iwo adzasula malupanga ao akhale zolimira, ndi nthungo zao zikhale anangwape; mtundu sudzanyamula lupanga kumenyana ndi mtundu wina, ndipo sadzaphunziranso nkhondo.

5 Inu a nyumba ya Yakobo, tiyeni, tiyende m'kuwala kwa Yehova.

6 Cifukwa inu mwasiya anthu anu a nyumba ya Yakobo, cifukwa kuti iwo adzazidwa ndi miyambo ya kum'mawa, ndipo ali olaula ngati Afilisti, naomba m'manja ndi ana a acilendo.

7 Dziko lao ladzala siliva ndi golidi, ngakhale cuma cao ncosawerengeka; dziko lao lidzalanso akavalo, ngakhale magareta ao ngosawerengeka.

8 Dziko lao ladzalanso mafano; iwo apembedza nchito ya manja ao ao, imene zala zao zao zinaipanga.

9 Munthu wacabe agwada pansi, ndi munthu wamkuru adzicepetsa, koma musawakhululukire.

10 Lowa m'phanga, bisala m'pfumbi, kucokera pa kuopsya kwa Yehova, ndi pa ulemerero wacifumu wace.

11 Maso a munthu akuyang'anira kumwamba adzatsitsidwa, ndi kudzikweza kwa anthu kudzaweramitsidwa pansi; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.

12 Cifukwa padzakhala tsiku la Yehova wa makamu pa zonse zonyada ndi zakudzikuza, ndi pa zonse zotukulidwa; ndipo zidzatsitsidwa;

13 ndi pa mitengo yonse yamkungudza ya Lebano, yaitari ndi yotukulidwa, ndi pa mitengo yonse yathundu ya Basana;

14 ndi pa mapiri onse atari, ndi pa zitunda zonse zotukulidwa;

15 ndi pa nsanja zazitari zonse, ndi pa macemba onse;

16 ndi pa ngalawa zonse za Tarisi, ndi pa zithunzithunzi zonse zokondweretsa.

17 Ndipo kudzikweza kwa munthu kudzaweramitsidwa pansi, kudzikuza kwa munthu kudzatsitsidwa; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.

18 Ndimo mafano adzapita psiti.

19 Anthu adzalowa m'mapanga a m'matanthwe, ndi m'maenje apansi, kuthawa kuopsya kwa Yehova, ndi ulemerero wacifumu wace, podzuka Iye kugwedeza dziko ndi mphamvu.

20 Tsiku limenelo munthu adzataya ku mfuko ndi ku mileme mafano ace asiliva ndi agolidi amene anthu anampangira iye awapembedze;

21 kuti akalowe m'mapanga a m'matanthwe, ndi m'mindala a m'miyala, kuthawa kuopsya kwa Yehova, ndi ulemerero wacifumu wace, podzuka Iye kugwedeza dziko ndi mphamvu,

22 Siyani munthu, amene mpweya wace uli m'mphuno mwace; cifukwa m'mene awerengedwamo ndi muti?

3

1 Ndipo onani, Ambuye, Yehova wa makamu, wacotsa ku Yerusalemu ndi ku Yuda mcirikizo wocirikiza cakudya conse ndi madzi onse, zimene zinali mcirikizo;

2 munthu wamphamvu, ndi munthu wankhondo; woweruza, ndi mneneri, ndi waula, ndi nkhalamba;

3 kapitao wa makumi asanu, ndi munthu wolemekezeka, ndi mphungu, ndi mmisiri waluso, ndi wodziwa matsenga.

4 Ndipo ndidzapereka ana, kuti akhale akuru ao, mwacibwana adzawalamulira.

5 Ndi anthu adzabvutidwa, yense ndi wina, yense ndi mnansi wace; mwana adzadzinyaditsa yekha pa akuru, ndi onyozeka pa olemekezedwa.

6 Pamene mwamuna adzamgwira mbale wace m'nyumba ya atate wace, nadzati, Iwe uli ndi cobvala, khala wolamulira wathu, ndi kupasula kumeneku kukhale m'dzanja lako;

7 tsiku limenelo adzakweza mau ace, kuti, Sindine wociritsa, cifukwa kuti m'nyumba mwanga mulibe cakudya kapena cobvala; inu simudzandiyesa ine wolamulira anthu.

8 Cifukwa kuti Yerusalemu wapasulidwa, ndi Yuda wagwa; cifukwa kuti lilume lao ndi macitidwe ao akana Yehova, kuti autse mkwiyo wa m'maso a ulemerero wace.

9 Maonekedwe a nkhope zao awacitira iwo mboni; ndipo amaonetsa ucimo wao monga Sodomu, saubisa. Tsoka kwa moyo wao! cifukwa iwo anadzicitira zoipa iwo okha.

10 Nenani za wolungama, kuti kudzamkomera iye; cifukwa oterowo adzadya zipatso za macitidwe ao.

11 Tsoka kwa woipa! kudzamuipira; cifukwa kuti mphotho ya manja ace idzapatsidwa kwa iye.

12 Anthu anga awabvuta ndi ana, awalamulira ndi akazi. Anthu anga inu, iwo amene akutsogolerani, ndiwo akucimwitsani, naononga njira zanu zoyendamo.

13 Yehova aimirira kuti atsutsane, naimiriranso kuti aweruze mitundu ya anthu.

14 Yehova adzalowa monenera mirandu ndi okalamba a anthu ace, ndi akuru ace: Ndinu amene mwadya munda wamphesa, zofunkha za waumphawi ziri m'nyumba zanu;

15 muti bwanji inu, amene mupsinja anthu anga, ndi kupera nkhope ya wosauka? ati Ambuye Yehova wa makamu.

16 Komanso Yehova ati, Cifukwa kuti ana akazi a Ziyoni angodzikuza atakweza makosi ao, ndi maso ao adama nayenda nanyang'ama poyenda pao naliza zigwinjiri za mapazi ao;

17 cifukwa cace Ambuye adzacita nkanambo pa liwombo la ana akazi a Ziyoni, ndipo Yehova adzabvundukula m'cuuno mwao.

18 Tsiku limenelo Ambuye adzacotsa zigwinjiri zao zokoma, ndi zitunga, ndi mphande;

19 mbera, ndi makoza, ndi nsaru za pankhope;

20 ndi zisada, ndi maunyolo a kumwendo, ndi mipango, ndi nsupa zonunkhira, ndi mphinjiri;

21 mphete, ndi zipini;

22 malaya a paphwando, ndi zopfunda, ndi zimbwi, ndi timatumba;

23 akalirole, ndi nsaru zabafuta, ndi nduwira, ndi zophimba.

24 Ndipo padzakhala m'malo mwa zotsekemera mudzakhala zobvunda; ndi m'malo mwa lamba cingwe; ndipo m'malo mwa tsitsi labwino dazi; m'malo mwa cobvala ca pacifuwa mpango waciguduli; zipsera m'malo mwa ukoma.

25 Amuna ako adzagwa ndi lupanga, ndi wamphamvu wako m'nkhondo.

26 Ndipo zipata zace zidzalira maiko; ndipo iye adzakhala bwinja, nadzakhala pansi.

4

1 Ndipo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi tsiku limenelo, nati, Ife tidzadya cakudya cathu cathu ndi kubvala zobvala zathu zathu; koma tichedwe dzina lako; cotsa citonzo cathu.

2 Tsiku limenelo mphukira ya Yehova idzakhala yokongola ndi ya ulemerero, cipatso ca nthaka cidzakhala cokometsetsa ndi cokongola, kwa iwo amene adzapulumuka a Israyeli.

3 Ndipo padzakhala, kuti iye amene asiyidwa m'Ziyoni, ndi iye amene atsala m'Yerusalemu, adzachedwa woyera; ngakhale yense amene walembedwa mwa amoyo m'Yerusalemu;

4 pamene Ambuye adzasambitsa litsiro la ana akazi a Ziyoni, nadzatsuka mwazi wa Yerusalemu, kucokera pakatipo, ndi mzimu wa ciweruziro, ndi mzimu wakutentha.

5 Ndipo Yehova adzalenga pokhala ponse pa phiri la Ziyoni, ndi pa masonkhano ace, mtambo ndi utsi usana, ndi kung'azimira kwa malawi a moto usiku; cifukwa kuti pa ulemerero wonse padzayalidwa cophimba.

6 Ndipo padzakhala cihema ca mthunzi, nthawi ya usana yopewera kutentha, pothawira ndi pousa mvula ndi mphepo.

5

1 Ndiyimbire wokondedwa wanga nyimbo ya wokondedwa wanga ya munda wace wamphesa, Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa m'citunda ca zipatso zambiri;

2 ndipo iye anakumba mcerenje kuzungulira kwete, natolatola miyala pamenepo naokapo mpesa wosankhika, namangapo pakati pace nsanja, nasema mopondera mphesa, nayembekeza kuti udzabala mphesa, koma unangobala mphesa zosadya.

3 Ndipo tsopano, inu okhala m'Yerusalemu, ndi anthu a Yuda, weruzanitu mlandu wa ine ndi munda wanga wamphesa.

4 Ndikanacitanso ciani ndi munda wanga wamphesa, cimene sindinacite m'menemo; muja ndinayembekeza kuti udzabala mphesa, wabaliranji mphesa zosadya?

5 Ndipo tsopano ndidzakuuzani cimene nditi ndicite ndi munda wanga wamphesa; ndidzacotsapo chinga lace, ndipo zidzadyedwa; ndidzagumula linga lace, ndipo zidzapondedwa pansi;

6 ndipo ndidzaupasula; sudzadzomboleredwa kapena kulimidwa; koma padzamera lunguzi ndi minga; ndidzalamuliranso mitambo kuti isabvumbwepo mvula.

7 Cifukwa kuti munda wamphesa wa Yehova wa makamu ndiwo banja la Israyeli, ndi anthu a Yuda, mtengo wace womkondweretsa; Iye anayembekeza ciweruziro, koma onani kuphana; nayembekeza cilungamo, koma onani kupfuula.

8 Tsoka kwa iwo amene aphatikiza nyumba ndi nyumba, amene alumikiza munda ndi munda, kufikira padzapanda malo, ndipo inu mudzasiyidwa nokha pakati pa dziko!

9 M'makutu anga, ati Yehova wa makamu, Zoonadi nyumba zambiri zidzakhala bwinja, ngakhale zazikuru ndi zokoma zopanda wokhalamo.

10 Cifukwa kuti munda wamphesa wa madera khumi udzangobala mbiya imodzi, ndi mbeu za nsengwa khumi zidzangobala nsengwa imodzi.

11 Tsoka kwa iwo amene adzuka m'mamawa kuti atsate zakumwa zaukali; amene acezera usiku kufikira vinyo awaledzeretsal

12 Ndipo zeze ndi mgoli, ndi lingaka ndi citoliro, ndi vinyo, ziri m'mapwando ao; koma iwo sapenyetsa nchito ya Yehova; ngakhale kuyang'ana pa macitidwe a manja ace.

13 Cifukwa cace anthu anga amuka m'nsinga, cifukwa ca kusowa nzeru; ndi amuna ao olemekezeka ali ndi njala, ndi khamu lao lauma kukhosi.

14 Ndipo manda akuza cilakolako cace, natsegula kukamwa kwace kosayeseka; ndi ulemerero wao, ndi unyinji wao, ndi phokoso lao, ndi iye amene akondwerera mwa iwo atsikira mommo.

15 Munthu wonyozeka waweramitsidwa, ndi munthu wochuka watsitsidwa, ndi maso a wodzikweza atsitsidwa;

16 koma Yehova wa makamu wakwezedwa m'ciweruziro, ndipo Mulungu Woyera wayeretsedwa m'cilungamo.

17 Pamenepo ana a nkhosa adzadyapo ngati m'busa mwao, ndi malo a bwinja a zonenepa zacilendo zidzadyapo.

18 Tsoka kwa iwo amene akoka mphulupulu ndi zingwe zacabe, ndi cimo ngati ndi cingwe ca gareta;

19 amene ati, Mlekeni iye akangaze, mlekeni iye afulumize nchito yace kuti ife tione; ndipo lekani uphungu wa Woyera wa Israyeli uyandikire, udze kuti tiudziwe!

20 Tsoka kwa iwo amene ayesa zoipa zabwino, ndi zabwino zoipa; amene aika mdima m'malo mwa kuyera, ndi kuyera m'malo mwa mdima; amene aika zowawa m'malo mwa zotsekemera, ndi zotsekemera m'malo mwa zowawa!

21 Tsoka kwa iwo amene adziyesera anzeru ndi ocenjera!

22 Tsoka kwa iwo amene ali a mphamvu yakumwa vinyo, ndi anthu olimba akusanganiza zakumwa zaukali;

23 amene alungamitsa woipa pa cokometsera mlandu, nacotsera wolungama cilungamo cace!

24 Cifukwa cace monga ngati lilime la moto likutha ciputu, ndi monga udzu wouma ugwa pansi m'malawi, momwemo muzu wao udzakhala monga wobvunda, maluwa ao adzauluka m'mwamba ngati pfumbi; cifukwa kuti iwo akana cilamulo ca Yehova wa makamu, nanyoza mau a Woyera wa Israyeli.

25 Cifukwa cace mkwiyo wa Yehova wayaka pa anthu ace, ndipo Iye watambasulira iwo dzanja lace, nawakantha, ndipo zitunda zinanthunthumira, ndi mitembo yao inali ngati zinyatsi pakati pa makwalala. Mwa izi zonse mkwiyo wace sunacoke, koma dzanja lace liri citambasulire.

26 Ndipo Iye adzakwezera a mitundu yakutari mbendera, nadzawayimbira mluzu, acokere ku malekezero a dziko; ndipo taonani, iwo adzadza ndi liwiro msanga msanga;

27 palibe amene adzalema, kapena adzapunthwa mwa iwo, palibe amene adzaodzera kapena kugona tulo; ngakhale lamba la m'cuuno mwao silidzamasuka, kapena comangira ca nsapato zao sicidzaduka;

28 amene mibvi yao ili yakuthwa, ndi mauta ao onse athifuka; ziboda za akavalo ao zidzayesedwa ngati mwala, ndi njinga zao ngati kabvumvulu;

29 kubangula kwao kudzafana ndi mkango, iwo adzabangula ngati ana a mikango, inde iwo adzabangula, nadzagwira nyama, naicotsa bwino opanda wakupulumutsa.

30 Ndipo iwo adzawabangulira tsiku limenelo ngati kukokoma kwa nyanja; ndipo wina ayang'ana padziko, taonani mdima ndi nsautso, kuyera kwadetsedwanso m'mitambo yace.

6

1 Caka cimene mfumu Uziya anafa, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando wacifumu wautari, ndi wotukulidwa, ndi zobvala zace zinadzala m'Kacisi.

2 Pamwamba pa Iye panaima aserafi; yense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi; awiri anaphimba nao nkhope yace, awiri naphimba nao mapazi ace, awiri nauluka nao.

3 Ndipo wina anapfuula kwa mnzace, nati, Woyera, Woyera, Woyera, Yehova wa makamu; dziko lonse lapansi ladzala ulemerero wace.

4 Ndipo maziko a ziundo anasunthika ndi mau amene anapfuula, ndipo nyumba inadzazidwa ndi utsi.

5 Ndipo ine ndinati, Tsoka kwa ine! cifukwa ndathedwa; cifukwa ndiri munthu wa milomo yonyansa, ndikhala pakati pa anthu a milomo yonyansa; cifukwa kuti maso anga aona Mfumu, Yehova wa makamu.

6 Pompo anaulukira kwa ine mmodzi wa aserafi, ali nalo khala lamoto m'dzanja mwace, limene analicotsa ndi mbaniro pa guwa la nsembe;

7 nakhudza nalo kukamwa kwanga nati, Taona ici cakhudza milomo yako; ndipo mphulupulu zako zacotsedwa, zocimwa zako zaomboledwa.

8 Ndipo ndinamva mau a Ambuye akuti, Ndidzatumiza yani, ndipo ndani adzatimukira ife? Ndipo ine ndinati, Ndine pano; munditumize ine.

9 Ndipo Iye anati, Kauze anthu awa, Imvani inu ndithu, koma osazindikira; yang'anani inu ndithu, koma osadziwitsa.

10 Nenepetsa mtima wa anthu awa, lemeretsa makutu ao, nutseke maso ao; angaone ndi maso ao, angamve ndi makutu ao, angazindikire ndi mtima wao, nakabwerenso, naciritsidwe.

11 Pompo ndinati ine, Ambuye mpaka liti? Ndipo anayankha, Mpaka midzi ikhala bwinja, yopanda wokhalamo, ndi nyumba zopanda munthu, ndi dziko likhala bwinja ndithu,

12 ndipo Yehova wasunthira anthu kutari, ndi mabwinja adzacuruka pakati pa dziko.

13 Ndipo likatsala limodzi la magawo khumi m'menemo, lidzadyedwanso; monga kacere, ndi monganso thundu, imene tsinde lace likhalabe ataigwetsa; cotero mbeu yopatulika ndiyo tsinde lace.

7

1 Ndipo panali masiku a Ahazi, mwana wa Yotamu, mwana wa Uziya, mfumu ya Yuda, kuti Rezini, mfumu ya Aramu, ndi Peka, mwana wa Remaliya, mfumu ya Israyeli, anakwera kunka ku Yerusalemu, kumenyana nao; koma sanathe kuupamnana.

2 Ndipo anauza a nyumba ya Davide, kuti Aramu wapangana ndi Efraimu. Ndipo mtima wace unagwedezeka, ndi mtima wa anthu ace, monga mitengo ya m'nkhalango igwedezeka ndi mphepo.

3 Ndipo Yehova anati kwa Yesaya, Turuka tsopano kukacingamira Ahazi, iwe ndi Seariyasubu, mwana wamwamuna wako, pa mamariziro a mcerenje wa thamanda la pamtunda, ku khwalala la pa mwaniko wa wotsuka nsaru;

4 nukati kwa iye, Cenjera, khala ulipo; usaope, mtima wako usalefuke, cifukwa ca zidutswa ziwirizi za miuni yofuka, cifukwa ca mkwiyo waukali wa Rezini ndi Aramu, ndi wa mwana wa Remaliya.

5 Cifukwa Aramu ndi Efraimu, ndi mwana wa Remaliya anapangana kukucitira zoipa, nati,

6 Tiyeni, tikwere, timenyane ndi Yuda, timbvute; tiyeni, tidzigumulire mpata, pamenepo tikhazike mfumu pakati pace, ngakhale mwana wamwamuna wa Tabeeli;

7 atero Ambuye Yehova, Upo wao sudzaimai, sudzacitidwa.

8 Pakuti mutu wa Aramu ndi Damasiko, ndi mutu wa Damasiko ndi Rezini, zisadapite zaka makumi asanu ndi limodzi mphambu zisanu Efraimu adzatyokatyoka, sadzakhalanso mtundu wa anthu;

9 ndipo mutu wa Efraimu ndi Samariya, ndi mutu wa Samariya ndi mwana wa Remaliya, mukapanda kukhulupirira ndithu simudzakhazikika.

10 Ndipo Yehova ananenanso kwa Ahazi nati,

11 Udzipemphere wekha cizindikilo ca kwa Yehova Mulungu wako; pempha cam'mwakuya, kapena cam'mwamba.

12 Koma Ahazi anati, Sindipemphai ngakhale kumyesa Yehova.

13 Ndipo iye anati, Mverani inu tsopano, inu a nyumba ya Davide; kodi ndi kanthu kakang'ono kwa inu kutopetsa anthu, kuti inu mutopetsa Mulungu wanga?

14 Cifukwa cace Ambuye mwini yekha adzakupatsani inu cizindikilo; taonani namwali adzaima, nadzabala mwana wamwamuna, nadzamucha dzina lace Imanueli.

15 Iye adzadya mafuta ndi uci, pamene adziwa kukana coipa ndi kusankha cabwino.

16 Popeza kuti asanadziwe mwanayo kukana coipa ndi kusankha cabwino, dziko limene mafumu ace awiri udana nao lidzasyidwa.

17 Yehova adzatengera pa iwe, ndi pa anthu ako, ndi pa nyumba ya atate wako, masiku, akuti sanadze oterewa kuyambira tsiku limene Efraimu analekana ndi Yuda; kunena mfumu ya Asuri.

18 Ndipo padzakhala tsiku limenelo kuti Yehova adzayimbira mluzu cimphanga ciri m'mbali ya kumtunda kwa nyanja za Aigupto, ndi njuci iri m'dziko la Asuri.

19 Ndipo zidzafika nizitera zonse m'zigwa zabwinja, ndi m'maenje a matanthwe, ndi paminga ponse, ndi pamabusa ponse.

20 Tsiku limenelo Ambuye adzameta mutu, ndi ubweya wa m'mapazi, ndi lumo lobwereka liri tsidya lija la Nyanja, kunena mfumu ya Asuri; ndilo lidzamarizanso ndebvu.

21 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti munthu adzaweta ng'ombe yaikazi yaing'ono, ndi nkhosa ziwiri;

22 ndipo padzakhala, cifukwa ca kucuruka kwa mkaka umene zidzapatsa, iye adzadya mafuta; pakuti mafuta ndi uci adzadya yense wosiyidwa pakati pa dziko.

23 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti pali ponse panali mipesa cikwi cimodzi ya mtengo wace wa ndalama cikwi cimodzi, padzakhala lunguzi ndi minga.

24 Munthu adzafikako ndi mibvi ndi uta; pakuti dziko lonse lidzakhala la lunguzi ndi minga.

25 Ndipo zitunda zonse zinalimidwa ndi khasu, iwe sudzafikako cifukwa ca kuopa lunguzi ndi minga, koma pomwepo padzakhala potumizira ng'ombe ndi popondaponda nkhosa.

8

1 Ndipo Yehova anati kwa ine, Tenga iwe polembapo papakuru, nulembe pamenepo ndi malembedwe odziwika, Kangazakufunkha Fulumirakusakaza,

2 Ndipo ndidzadzitengera ine mboni zokhulupirika, Uriya wansembe, ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya.

3 Ndipo ndinanka kwa mneneri wamkazi; ndipo iye anatenga pakati nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, Uche dzina lace, Kangazakufunkha Fulumirakusakaza.

4 Cifukwa kuti mwana asakhale ndi nzeru yakupfuula, Atate wanga, ndi Amai wanga, cuma ca Damasiko ndi cofunkha ca Samariya cidzalandidwa pamaso pa mfumu ya Asuri.

5 Ndipo Yehova ananena kwa ine kaciwirinso, nati,

6 Popeza anthu awa akana madzi a Silowa, amene ayenda pang'ono pang'ono, nakondwerera mwa Rezini ndi mwa mwana wa Remaliya;

7 cifukwa cace, taonani, Ambuye atengera pa iwo madzi a Nyanja, olimba ndi ambiri, kunena mfumu ya Asuri ndi ulemerero wace wonse; ndipo iye adzadzala mphaluka zace zonse, nadzasefukira pamtunda ponse.

8 Ndipo iye adzapitapitakulowa m'Yuda; adzasefukira, napitirira; adzafikira m'khosi; ndi kutambasula kwa mapiko ace, kudzakwanira dziko lanu m'citando mwace, inu Imanueli.

9 Citani phokoso, anthu inu, koma mudzatyokatyoka; cherani khutu, inu nonse a maiko akutari; kwindani nokha, koma mudzatyokatyoka; kwindani nokha, koma mudzatyokatyoka.

10 Panganani upo, koma udzakhala cabe; nenani mau, koma sadzacitika; pakuti Mulungu ali pamodzi ndi ife.

11 Pakuti Yehova watero kwa ine ndi dzanja lolimba, nandilangiza ine kuti ndisayende m'njira ya anthu awa, nati,

12 Musacinene, Ciwembu; ciri conse cimene anthu awa adzacinena, Ciwembu; musaope monga kuopa kwao kapena musacite mantha.

13 Yehova wa makamu, Iye mudzamyeretsa; muope Iye, akucititseni mantha Iye.

14 Ndipo Iye adzakhala malo opatulika; koma mwala wopunthwitsa, ndi thanthwe lolakwitsa la nyumba zonse ziwiri za Israyeli, khwekhwe ndi msampha wa okhala m'Yerusalemu.

15 Ndipo ambiri adzapunthwapo, nagwa, natyoka, nakodwa, natengedwa.

16 Manga umboni, mata cizindikilo pacilamulo mwa aphunzi anga.

17 Ndipo ndidzalindira Yehova, amene wabisira a nyumba ya Yakobo nkhope yace, ndipo ndidzamyembekeza Iye,

18 Taonani, ine ndi ana amene Yehova wandipatsa ine, tiri zizindikilo ndi zodabwitsa mwa Israyeli, kucokera kwa Yehova wa makamu, amene akhala m'phiri la Ziyoni.

19 Ndipo pamene iwo adzati kwa iwe, Funa kwa olaula, ndi obwebweta, amene alira pyepye, nang'ung'udza; kodi anthu sadzafuna kwa Mulungu wao? Cifukwa ca amoyo, kodi adzafuna kwa akufa?

20 Kucilamulo ndi kuumboni! ngati iwo sanena malinga ndi mau awa, ndithu sadzaona mbanda kuca.

21 Ndipo iwo adzapitirira obvutidwa ndi anjala, ndipo padzakhala kuti pokhala ndi njala iwo adzadziputa okha, ndi kutemberera mfumu yao, ndi Mulungu wao; ndi kugadamira nkhope zao kumwamba;

22 nadzayang'ana padziko, koma taonani, nkhawa ndi mdima, kuziya kwa nsautso; ndi mdima woti bi udzaingitsidwa.

9

1 Koma kumene kunali nsautso sikudzakhala kuziya. Poyamba paja Mulungu ananyozetsa dziko la Zebuloni, ndi dziko la Naftali, koma potsiriza pace Iye analicitira ulemu, pa khwalala la kunyanja, patsidya pa Yordano, Galileya wa amitundu.

2 Anthu amene anayenda mumdima, aona kuwala kwakukuru; iwo amene anakhala m'dziko la mthunzi wa imfa, kuwala kwaturukira kwa iwo.

3 Inu mwacurukitsa mtundu, inu mwaenjezera kukondwa kwao; iwo akondwa pamaso panu monga akondwera m'masika, monga anthu akondwa pogawana zofunkha.

4 Pakuti gori la katundu wace, ndi mkunkhu wa paphewa pace, ndodo ya womsautsa, inu mwazityola monga tsiku la Midyani.

5 Pakuti zida zonse za mwamuna wobvala zida za nkhondo m'phokosomo, ndi zobvala zobvimvinika m'mwazi, zidzakhala zonyeka ngati nkhuni.

6 Pakuti kwa ife mwana wakhanda wabadwa, kwa ife mwana wamwamuna wapatsidwa; ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lace, ndipo adzamucha dzina lace Wodabwitsa, Wauphungu, Mulungu wamphamvu, Atate Wosatha, Kalonga wa mtendere.

7 Za kuenjezera ulamuliro wace, ndi za mtendere sizidzatha pa mpando wacifumu wa Davide, ndi pa ufumu wace, kuukhazikirsa, ndi kuucirikiza ndi ciweruziro ndi cilungamo kuyambira tsopano ndi kunkabe nthawi zonse. Cangu ca Yehova wa makamu cidzacita zimenezi.

8 Ambuye anatumiza mau kwa Yakobo, ndipo anatsikira pa Israyeli.

9 Ndipo anthu onse adzadziwa, ngakhale Efraimu ndi okhala m'Samariya, amene anena m'kunyada ndi m'kukula kwa mtima,

10 Njerwa zagwa, koma ife tidzamanga ndi miyala yosema; mikuyu yagwetsedwa, koma tidzaisinthanitsa ndi mikungudza.

11 Cifukwa cace Yehova adzamkwezera Rezini olimbana naye, nautsa adani ace;

12 Aramu patsogolo ndi Afilisti pambuyo; ndipo iwo adzadya Israyeli ndi kukamwa koyasama. Mwa izi zonse mkwiyo wace sunacoke, koma dzanja lace liri citambasulire.

13 Koma anthu sanatembenukire kwa Iye amene anawamenya, ngakhale kufuna Yehova wa makamu.

14 Cifukwa cace Yehova adzadula mutu wa Israyeli ndi mcira wace; nthambi ya kanjedza ndi mlulu, tsiku limodzi.

15 Nkhalamba ndi wolemekezeka ndiye mutu, ndi mneneri wophunzitsa zonama ndiye mcira.

16 Pakuti iwo amene atsogolera anthuwa, ndiwo awasokeretsa; ndipo iwo amene atsogoleredwa nao aonongeka.

17 Cifukwa cace Ambuye sadzakondwera ndi anyamata ao, ngakhale kuwacitira cifundo amasiye ao ana ndi akazi; popeza yense ali wodetsa ndi wocimwa, m'kamwa monse mulankhula zopusa. Mwa izi zonse mkwiyo wace sunacoke, koma dzanja lace liri citambasulire.

18 Pakuti kucimwa kwayaka ngati moto kumariza lunguzi ndi minga, inde kuyaka m'nkhalango ya m'thengo, ndipo zifuka capamwamba, m'mitambo yautsi yocindikira.

19 M'kukwiya kwa Yehova wa makamu, dziko latenthedwa ndithu, anthunso ali ngati nkhuni; palibe munthu wocitira mbale wace cisoni.

20 Ndipo wina adzakwatula ndi dzanja lamanja, nakhala ndi njala; ndipo adzadya ndi dzanja lamanzere, osakhutai; iwo adzadya munthu yense nyama ya mkono wace wa iye mwini.

21 Manase adzadya Efraimu ndi Efraimu adzadya Manase, ndipo iwo pamodzi adzadyana ndi Yuda. Mwa izi zonse mkwiyo wace sunacoke, koma dzanja lace liri citambasulire.

10

1 Tsoka kwa iwo amene alamulira malamulo osalungama, ndi kwa alembi olemba mphulupulu;

2 kuwapatulira osowa kuciweruziro, ndi kucotsera anthu anga aumphawi zoyenera zao, kuti alande za akazi amasiye, nafunkhire ana amasiye!

3 Ndipo mudzacita ciani tsiku lakudza woyang'anira, ndi cipasuko cocokera kutari? mudzathawira kwa yani kufuna kuthangatidwa? mudzasiya kuti ulemerero wanu?

4 Adzangoweramira pansi pa andende, ndipo adzagwa pansi pa ophedwa. Mwa izi zonse mkwiyo wace sunacoke, koma dzanja lace liri citambasulire.

5 Iwe Asuri cibonga ca mkwiyo wanga, ndodo m'dzanja lace muli ukali wanga!

6 Ine ndidzamtumiza kumenyana ndi mtundu wosalemekeza, ndi pa anthu a mkwiyo wanga ndidzamlangiza, kuti afunkhe, agwire zolanda, awapondereze pansi, monga dothi la pamakwalala.

7 Koma iye safuna cotero, ndipo mtima wace suganizira cotero, koma mtima wace ulikufuna kusakaza, ndi kuduladula amitundu osawerengeka.

8 Popeza ati, Akalonga anga kodi sali onse mafumu?

9 Kodi Kalino sali wonga ngati Karikemesi? kodi Hamati sali ngati Aripadi? kodi Samariya sali ngati Damasiko?

10 Popeza dzanja langa lapeza maufumu a mafano, mafano ao osema anapambana ndi iwo a ku Yerusalemu ndi ku Samariya;

11 monga ndacitira Samariya ndi mafano ace, momwemo kodi sindidzacitira Yerusalemu ndi mafano ace?

12 Cifukwa cace padzaoneka, kuti pamene Ambuye atatha nchito yace yonse pa phiri la Ziyoni ndi pa Yerusalemu, ndidzalanga zipatso za mtima wolimba wa mfumu ya Asuri, ndi ulemerero wa maso ace okwezedwa.

13 Popeza anati, Mwa mphamvu ya dzanja langa ndacita ici, ndi mwa nzeru yanga; pakuti ine ndiri wocenjera; ndacotsa malekezero a anthu, ndalanda cuma cao, ndagwetsa monga munthu wolimba mtima iwo okhala pa mipando yacifumu;

14 dzanja langa lapeza monga cisa, cuma ca mitundu ya anthu, ndipo monga munthu asonkhanitsa mazira osiyidwa, ine ndasonkhanitsa dziko lonse lapansi, ndipo panalibe cogwedeza phiko, kapena cotsegula pakamwa, kapena colira pyepye.

15 Kodi nkhwangwa idzadzikweza yokha, pa iye amene adula nayo? kodi cocekera cidzadzikweza cokha pa iye amene acigwedeza, ngati cibonga ingamgwedeze iye amene ainyamula, ngati ndodo inganyamule kanthu popeza iri mtengo.

16 Cifukwa cace Ambuye, Yehova wa makamu, adzarumiza kuonda mwa onenepa ace; ndipo pansi pa ulemerero wace padzayaka kutentha, konga ngati kutentha kwa moto.

17 Ndipo kuwala kwa Israyeli kudzakhala moto, ndi Woyera wace adzakhala lawi; ndipo lidzatentha ndi kuthetsa minga yace ndi lunguzi wace tsiku limodzi.

18 Ndipo adzanyeketsa ulemerero wa m'nkhalango yace, ndi wa m'munda wace wopatsa bwino, moyo ndi thupi; ndipo padzakhala monga ngati pokomoka wonyamula mbendera.

19 Ndipo mitengo yotsala ya m'nkhalango yace idzakhala yowerengeka, kuti mwana ailembera.

20 Ndipo padzakhala tsiku lomwelo, kuti otsala a Israyeli, ndi iwo amene anapulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzatsamiranso iye amene anawamenya; koma adzatsamira Yehova Woyera wa Israyeli, ntheradi.

21 Otsala adzabwera, otsala a Yakobo, kwa Mulungu wamphamvu.

22 Popeza ngakhale anthu anu Israyeli akunga mcenga wa kunyanja, otsala ao okha okha adzabwera; cionongeko catsimikizidwa, cilungamo cace cisefukira.

23 Pakuti Ambuye Yehova wa makamu adzacita cionongeko cotsimikizidwa pakati pa dziko lonse lapansi.

24 Cifukwa cace atero Ambuye; Yehova wa makamu, Inu anthu anga okhala m'Ziyoni, musaope Asuri; ngakhale amenya inu ndi cibonga, kapena kukusamulira iwe ndodo yace, monga amacitira Aigupto.

25 Pakuti patsala kamphindi, ndipo ukali udzathedwa ndi mkwiyo wanga wakuwaononga.

26 Ndipo Yehova wa makamu adzamuutsira cikoti, monga m'kuphedwa kwa Midyani pa thanthwe la Orebu; ndipo cibonga cace cidzakhala pamwamba pa nyanja, ndipo adzaisamula monga anacitira Aigupto,

27 Ndipo padzakhala tsiku lomwelo, kuti katundu wace adzacoka pa phewa lako, ndi gori lace pakhosi pako; ndipo gori lidzathedwa cifukwa ca kudzoza mafuta.

28 Wafika ku Aiati, wapitirira kunka ku Migroni; pa Mikimasi asunga akatundu ace;

29 wapita pampata; wagona pa Geba, Rama anthunthumira; Gibeya wa Sauli wathawa.

30 Pfuula ndi mau ako iwe mwana wamkazi wa Galimu! tamva, iwe Laisa! iwe Anatoti wosauka!

31 Madimena ali wothawathawa; okhala m'Gebimu asonkhanakutiathawe.

32 Lero lomwe adzaima pa Nobu; agwedezera dzanja lace pa phiri la mwana wamkazi wa Ziyoni, phiri la Yerusalemu.

33 Taonani, Ambuye Yehova wa makamu adzasadza nthambi moopsya; ndipo zazitari msinkhu zidzadulidwa, ndipo zazitari zidzagwetsedwa.

34 Ndipo adzadula nkhalango za m'thengo ndi citsulo, ndipo Lebano adzagwa ndi wamphamvu.

11

1 Ndipo padzaturuka mphukira pa tsinde la Jese, ndi nthambi yoturuka m'mizu yace idzabala zipatso;

2 ndipo mzimu wa Yehova udzambalira iye mzimu wanzeru ndi wakuzindikira, mzimu wa uphungu ndi mphamvu, mzimu wakudziwa ndi wakuopa Yehova;

3 ndipo adzakondwera nako kumuopa Yehova, ndipo sadzaweruza monga apenya maso, sadzadzudzula mwamphekesera:

4 koma ndi cilungamo adzaweruza aumphawi, nadzadzudzulira ofatsa a m'dziko moongoka; ndipo adzamenya dziko lapansi ndi cibonga ca kukamwa kwace, nadzapha oipa ndi mpweya wa milomo yace.

5 Ndipo cilungamo cidzakhala mpango wa m'cuuno mwace, ndi cikhulupiriko cidzakhala mpango wa pa zimpsyo zace.

6 Mmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wa nkhosa, ndipo nyalugwe adzagona pansi ndi mwana wa mbuzi; ndipo mwana wa ng'ombe ndi mwana wa mkango ndi coweta conenepa pamodzi; ndipo mwana wamng'ono adzazitsogolera.

7 Ndipo ng'ombe yaikazi ndi cirombo zidzadya pamodzi; ndipo ana ao ang'ono adzagona pansi; ndipo mkango udzadya udzu ngati ng'ombe.

8 Ndipo mwana wakuyamwa adzasewera pa una wa mamba, ndi mwana woleka kuyamwa adzaika dzanja lace m'pfunkha la mphiri.

9 Sizidzaipitsa, sizidzasakaza m'phiri langa lonse loyera, cifukwa kuti dziko lapansi lidzadzala ndi odziwa Yehova, monga mdazi adzaza nyanja.

10 Ndipo padzakhala tsiku lomwelo, kuti muzu wa Jese umene uima ngati mbendera ya mitundu ya anthu, amitundu adzafunafuna uwu; ndipo popuma pace padzakhala ulemerero.

11 Ndipo padzakhala tsiku lomwelo, kuti Ambuye adzabweza kaciwiri ndi dzanja lace anthu ace otsala ocokera ku Asuri, ndi ku Aigupto, ndi ku Patirosi, ndi ku Kusi, ndi ku Elamu, ndi ku Sinara, ndi ku Hamati, ndi ku zisumbu za m'nyanja yamcere.

12 Ndipo Iye adzaimika mbendera ya amitundu, ndipo adzasonkhanitsa oingitsidwa a Israyeli, namema obalalika a Yuda, kucokera ku madera anai a dziko lapansi.

13 Ndipo nsanje ya Efraimu idzacoka, ndi iwo amene abvuta Yuda adzadulidwa; Efraimu sacitira nsanje Yuda, ndi Yuda sacitira nsanje Efraimu.

14 Ndipo adzagudukira mapewa a Afilisti kumadzulo; pamodzi adzafunkha ana a kum'mawa; adzatambasula dzanja lao pa Edomu ndi pa Moabu; ndipo ana a Amoni adzawamvera.

15 Ndipo Yehova adzaononga ndithu bondo la nyanja ya Aigupto; ndipo ndi mphepo yace yopsereza adzagwedeza dzanja lace pa Nyanja, ndipo adzaimenya ikhale mphaluka zisanu ndi ziwiri, nadzaolotsa anthu pansi pouma.

16 Ndipo padzakhala khwalala la anthu ace otsala ocokera ku Asuri; monga lija la Israyeli tsiku lokwera iwo kuturuka m'dziko la Aigupto.

12

1 Tsiku lomwelo udzati, Ndikuyamikani inu Yehova; pakuti ngakhale munandikwiyira, mkwiyo wanu wacoka, ndipo mutonthoza mtima wanga.

2 Taonani, Mulungu ndiye cipulumutso canga; ndidzakhulupira, sindidzaopa; pakuti Yehova Mwini ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Iye ndiye cipulumutso canga.

3 Cifukwa cace mudzakondwera pakutunga madzi m'zitsime za cipulumutso.

4 Tsiku lomwelo mudzati, Muyamikire Yehova, bukitsani dzina lace, mulalikire macitidwe ace mwa mitundu ya anthu, munene kuti dzina lace lakwezedwa.

5 Muyimbire Yehova; pakuti wacita zaulemerero; cidziwike ici m'dziko lonse.

6 Tapfuula, takuwa iwe, wokhala m'Ziyoni, cifukwa Woyera wa Israyeli wa m'kati mwako ali wamkuru.

13

1 Katundu wa Babulo, imene anaiona Yesaya mwana wa Amozi.

2 Kwezani mbendera pa phiri loti se, kwezani mau kwa iwo, kodolani kuti alowe m'zipata za akuru.

3 Ine ndalamulira opatulidwa anga, inde, ndaitana amphamvu anga, acite mkwiyo wanga, okondwerera ndi ukuru wanga.

4 Mau a khamu m'mapiri, akunga amtundu waukuru wa anthu, mau a phokoso la maufumu a mitundu yosonkhanidwa! Yehova wa makamu asonkhanitsa khamu kunkhondo.

5 Acokera m'dziko lakutari, ku malekezero a thambo, ngakhale Yehova, ndi zida za mkwiyo wace, kuti aononge dziko lonse.

6 Kuwani inu; pakuti tsiku la Yehova liri pafupi; lidzafika monga cionongeko cocokera kwa Wamphamvuyonse.

7 Cifukwa cace manja onse adzafoka, ndi mitima yonse ya anthu idzasungunuka;

8 ndipo adzaopa; zowawa ndi masauko zidzawagwira; ndipo adzamva zowawa, ngati mkazi wakubala; adzazizwa wina ndi wina; nkhope zao zidzanga malawi a moto.

9 Taonani tsiku la Yehova lidza, lankhanza, ndi mkwiyo ndi kukalipira kwaukali; kupasula dziko, ndi kudzaonongamo akucimwa psiti.

10 Cifukwa nyenyezi za kumwamba ndi makamu ao sizidzawala; dzuwa lidzada m'kuturuka kwace, ndipo mwezi sudzaonetsa kuwala kwace.

11 Ndipo ndidzalanga dziko lapansi, cifukwa ca kuipa kwao, ndi oipa cifukwa ca mphulupulu zao; ndipo ndidzaletsa kudzikuza kwa onyada, ndidzagwetsa kudzikweza kwa oopsya.

12 Ndipo ndidzacepsa anthu koposa golidi, ngakhale anthu koposa golidi weniweni wa ku Ofiri.

13 Cifukwa cace ndidzanthunthumiritsa miyamba, ndipo dziko lapansi lidzagwedezeka kucokera m'malo ace, m'mkwiyo wa Yehova wa makamu, tsiku la mkwiyo wace waukali.

14 Ndipo padzakhala kuti monga mbawala yothamangitsidwa, ndi monga nkhosa zosazisonkhanitsa anthu, adzatembenukira yense kwa anthu ace, nathawira yense ku dziko lace.

15 Onse opezedwa adzapyozedwa, ndi onse ogwidwa adzagwa ndi lupanga.

16 Makanda ao adzatswanyidwe pamaso pao; m'nyumba mwao mudzafunkhidwa, ndi akazi ao adzakakamizidwa.

17 Taonani, ndidzawautsira Amedi, amene sadzasamalira siliva, ngakhale golidi sadzakondwera naye.

18 Mauta ao adzatha anyamata; ndipo sadzacitira cisoni cipatso ca mimba; diso lao silidzaleka ana.

19 Ndipo Babulo, ulemerero wa maufumu, mudzi wokongolawo Akasidi anaunyadira, adzakhala monga momwe Mulungu anapasula Sodomu ndi Gomora.

20 Anthu sadzakhalamo konse, sadzakhalamo mbadwo ndi mbadwo; M-arabu sadzamanga hema wace pamenepo; abusa sadzagonetsa makamu ao kumeneko.

21 Koma zirombo za m'cipululu zidzagona pamenepo; nyumba zao zidzadzala ndi zakukuwa; ndipo nthiwatiwa zidzakhala pamenepo, ndipo atonde adzajidimuka pamenepo,

22 Ndipo mimbulu idzalira m'maboma ao, ndi ankhandwe m'manyumba ao abwino; ndi nthawi yace iyandikira, ndi masiku ace sadzacuruka.

14

1 Pakuti Ambuye adzamcitira cifundo Yakobo, ndipo adzasankhanso Israyeli, ndi kuwakhazikitsa m'dziko la kwao; ndipo acilendo adzadziphatika okha kwa iwo, nadzadzigumikiza ku nyumba ya Yakobo.

2 Ndipo mitundu ya anthu idzawatenga, ndi kuwafikitsa ku malo a kwao; ndipo a nyumba ya Israyeli adzakhala nao amitunduwo m'dziko la Yehova, ndi kuwayesa atumiki ndi adzakazi, ndipo amitunduwo adzatengedwa ndende, ndi amenewo anali ndende zao; ndipo Aisrayeli adzalamulira owabvuta.

3 Ndipo padzakhala tsiku loti Yehova adzakupumitsa cisoni cako, ndi nsautso yako, ndi nchito yako yobvuta, imene anakugwiritsa,

4 pamenepo udzayimbira mfumu ya ku Babulo nyimbo iyi yancinci, ndi kuti, Wobvuta wathadi! mudzi wagolidi wathadi!

5 Yehova watyola mkunkhu wa woipa, ndodo yacifumu ya wolamulira.

6 Wokantha anthu mwaukali kuwakantha cikanthire, wolamulira amitundu mokwiya, angosautsidwa wopanda womlanditsa.

7 Dziko lonse lapuma, liri du; iwo ayamba kuyimba nyimbo,

8 Inde, milombwa ikondwera ndi iwe, ndi mikungudza ya Lebano, ndi kunena, Cigwetsere iwe pansi, palibe wokwera kudzatidula ife.

9 Kunsi kwa manda kugwedezeka, cifukwa ca iwe, kukucingamira podza pako; kukuutsira iwe mizimu, ngakhale onse akuru akuru a dziko lapansi; kukweza kucokera m'mipando yao mafumu onse a amitundu.

10 Onse adzabvomera, nadzati kwa iwe, Kodi iwe wakhalanso wopanda mphamvu ngati ife? kodi iwe wafanana nafe?

11 Cifumu cako catsitsidwa kunsi ku manda, ndi phokoso la mingoli yako; mbozi zayalidwa pansi pa iwe, ndi mphukutu zakukuta.

12 Wagwadi kucokera kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mbanda kuca! Wagwetsedwa pansi, iwe wolefula amitundu!

13 Ndipo iwe unati mumtima mwako, Ndidzakwera kumwamba, ndidzakweza mpando wanga wacifumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pamwamba pa phiri la khamu, m'malekezero a kumpoto;

14 ndidzakwera pamwamba pa mitambo, ndidzafanana ndi Wam'mwambamwamba.

15 Koma udzatsitsidwa kunsi ku manda, ku malekezero a dzenje.

16 Iwo amene akuona iwe adzayang'anitsitsa iwe, nadzalingalira za iwe, ndi kuti, Kodi uyu ndi munthu amene ananthunthumiritsa dziko lapansi, amene anagwedeza maufumu;

17 amene anapululutsa dziko, napasula midzi yace, amene sanamasula ndende zace, zinke kwao?

18 Mafumu onse a amitundu, onsewo agona m'ulemerero yense kunyumba kwace.

19 Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yonyansa, ngati cobvala ca ophedwa, opyozedwa ndi lupanga, otsikira ku miyala ya dzenje, monga ngati mtembo wopondedwa ndi phazi.

20 Iwe sudzaphatikizidwa pamodzi nao poikidwa, pakuti iwe waononga dziko lako, wapha anthu ako; mbeu ya ocita zoipa sidzachulidwa konse.

21 Konzani inu popherapo ana ace, cifukwa ca kuipa kwa atate ao; kuti iwo asadzauka ndi kukhala nalo dziko, ndi kudzaza dziko lapansi ndi midzi.

22 Ndipo Ine ndidzawaukira, ati Yehova wa makamu, ndi kuononga ku Babulo dzina ndi otsala, ndi mwana wamwamuna, ndi cidzukulu cacimuna, ati Yehova.

23 Ndidzayesapo pokhala nungu, ndi madziwe a madzi; ndipo ndidzasesapo ndi tsace la cionongeko, ati Yehova wa makamu.

24 Yehova wa makamu walumbira, nati, Ndithu monga ndaganiza, cotero cidzacitidwa; ndipo monga ndapanga uphungu, cotero cidzakhala;

25 kuti Ine ndidzatyola Asuri m'dziko langa, ndi pamwamba pa mapiri anga ndidzawapondereza; pomwepo gori lace lidzacoka pa iwo, ndi katundu wace adzacoka paphuzi pao.

26 Umenewu ndi uphungu wopangira dziko lonse; ndipo ili ndi dzanja lotambasulidwa pa amitundu onse.

27 Pakuti Yehova wa makamu wapanga uphungu, ndani adzauleketsa? ndi dzanja lace latambasulidwa, ndani adzalibweza?

28 Caka cimene mfumu Ahazi anamwalira katundu amene analipo.

29 Usakondwere, lwe Filistia, wonsewe, potyoka ndodo inakumenya; pakuti m'muzu wa njoka mudzaturuka mphiri, ndimo cipatso cace cidzakhala njoka yamoto youluka.

30 Ndi oyamba kubadwa a osauka adzadya, aumphawi nadzagona pansi osatekeseka; ndipo ndidzapha muzu wako ndi njala, ndi otsala ako adzaphedwa.

31 Lira, cipata iwe; pfuula, mudzi iwe; wasungunuka, Filistia wonsewe, pakuti utsi ucokera kumpoto, ndipo palibe wosokera m'mizere yace.

32 Ndipo adzayankhanji amithenga a amitundu? Kuti Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo m'menemo anthu ace obvutidwa adzaona pobisalira.

15

1 Katundu wa Moabu. Pakuti usiku umodzi Ara wa ku Moabu wapasuka, nakhala cabe; usiku umodzi Kiri wa Moabu wapasuka, nakhala cabe.

2 Akwera kukacisi, ndi ku Dibo, kumisanje, kukalira; pa Nebo ndi pa Medeba a Moabu pali kulira; pamitu pao ponse pali dazi, ndebvu zonse zametedwa.

3 M'makwalala mwao adzimangira ciguduli m'cuuno, pamwamba pa nyumba zao, ndi m'malo a mabwalo ao, yense akuwa, naliritsa kwambiri.

4 Ndi Hesiboni apfuula zolimba, ndi Eliale; mau ao amveka, ngakhale ku Yahazi; cifukwa cace amuna ankhondo a Moabu apfuula zolimba; moyo wace wanthunthumira m'kati mwace.

5 Mtima wanga upfuula cifukwa ca Moabu: akuru ace athawira ku Zoari, ku Eglatiselisiya; pakuti pa cikweza ca Luhiti akwera alikulira, pakuti m'njira ya Horanaimu akweza mpfuu wa cionongeko.

6 Pakuti pa madzi a Nimirimi padzakhala mabwinja; papeza udzu wafota, msipu watha.

7 Cifukwa cace zocuruka adazipeza, ndi zosungidwa zao adzazitenga kunka nazo ku mtsinje wa mabango.

8 Pakuti kulira kwamveka kuzungulira malire a Moabu; kukuwa kwace kwafikira ku Eglaimu, ndi kukuwa kwace kwafikira ku Beerelimu.

9 Pakuti madzi a Dimoni adzala mwazi; pakuti ndidzatengera zina pa! Dimoni, mkango pa iye amene anapulumuka ku Moabu, ndi pa otsala am'dziko.

16

1 Tumizani inu ana a nkhosa kwa wolamulira wa dziko kucokera ku Sela kunka kucipululu, mpaka ku phiri la mwana wamkazi wa Ziyoni.

2 Pakuti ana akazi a Moabu adzakhala pa madooko a Arinoni, ngati mbalame zoyendayenda, ngati cisa cofwancuka.

3 Citani uphungu, weruzani ciweruziro; yesa mthunzi wako monga usiku pakati pa usana; bisa opitikitsidwa, osaulula woyendayenda.

4 Opitikitsidwa a Moabu akhale ndi iwe, khala iwe comphimba pamaso pa wofunkha; pakuti kumpambapamba kwalekeka, kufunkha kwatha, opondereza atsirizika m'dziko.

5 Ndipo mpando wacifumu udzakhazikika m'cifundo, ndimo wina adzakhala pamenepo m'zoona, m'cihema ca Davide, nadzaweruza, nadzafunitsa ciweruziro, nadzafulumira kucita cilungamo.

6 Ife tinamva kunyada kwa Moabu, kuti iye ali wonyada ndithu; ngakhale kudzitama kwace, ndi kunyada kwace ndi mkwiyo wace; matukutuku ace ali acabe.

7 Cifukwa cace Moabu adzakuwa cifukwa ca Moabu, onse adzakuwa; cifukwa ca maziko a Kirihareseti mudzalira maliro, osautsidwa ndithu.

8 Pakuti minda ya ku Hesiboni yalefuka, ndi mpesa wa ku Sibimai; ambuye a mitundu atyolatyola mitengo yosankhika yace; iwo anafikira ngakhale ku Yazeri, nayendayenda m'cipululu; nthambi zace zinatasa, zinapitima panyanja.

9 Cifukwa cace ndidzalira ndi kulira kwa Yazeri, cifukwa ca mpesa wa Sibima, ndidzakukhathamiza ndi misozi yanga, iwe Hesiboni ndi Eleale; cifukwa kuti pa zipatso zako za malimwe, ndi pa masika ako, mpfuu wankhondo wagwera.

10 Ndipo cikondwero ndi msangalalo zacotsedwa m'munda wapatsa zipatso; ndi m'minda ya mipesa simudzakhala kuyimba, ngakhale phokoso losangalala; palibe woponda adzaponda vinyo m'moponderamo; ndaleketsa mpfuu wa masika amphesa.

11 Cifukwa cace m'mimba mwanga mulirira Moabu, ngati mngoli, ndi za m'mtima mwanga zilirira Kiriheresi.

12 Ndipo padzakhala kuti pamene Moabu adzadzionetsa yekha, ndi kudzitopetsa pamsanje, ndipo kufika ku malo ace oyera kudzapemphera, sadzapindulapo kanthu.

13 Awa ndi mau amene Yehova adanena za Moabu nthawi zapitazo.

14 Koma tsopano Yehova wanena, nati, Zisanapite zaka zitatu monga zaka za wolembedwa nchito, ulemerero wa Moabu udzakhala wonyozeka, ndi khamu lalikuru lace, ndi otsala adzakhala ang'ongong'ono ndi acabe.

17

1 Katundu wa Damasiko. Taonani, Damasiko wacotsedwa usakhalenso mudzi, ndimo udzangokhala muunda wopasudwa.

2 Midzi ya Aroeri yasiyidwa; idzakhala ya zoweta zogona pansi, opanda woziopsya.

3 Ku Efraimu sikudzakhalanso linga, ngakhale ufumu ku Damasiko, ngakhale otsala kwa Aramu; iwo adzakhala ngati ulemerero wa ana a Israyeli, ati Yehova wamakamu.

4 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti ulemerero wa Yakobo udzakhala wopyapyala, ndi kunenepa kwa thupi lace kudzaonda.

5 Ndipo padzakhala ngati wamasika alikumweta tirigu wosaceka, ndi dzanja lace lirikudula ngala; inde padzakhala ngati pamene wina akunkha ngala m'cigwa ca Refaimu.

6 Koma mudzasiyidwa m'menemo khunkha, monga ngati kugwedeza kwace kwa mtengo waazitona, zipatso ziwiri pena zitatu m'nsonga ya nthambi yosomphoka, zinai pena zisanu m'nthambi za kunthemba, za mtengo wobalitsa, ati Yehova, Mulungu wa Israyeli.

7 Tsiku limenelo munthu adzayang'ana kwa Mlengi wace, ndipo maso ace adzalemekeza Woyera wa Israyeli.

8 Ndipo iye sadzayang'ana pa maguwa a nsembe, nchito ya manja ace, ngakhale kulemekeza cimene anacipanga ndi zala zace, ngakhale zifanizo pena mafano a dzuwa.

9 Tsiku limenelo midzi yace yolimba idzakhala ngati mabwinja a m'nkhalango, ndi a pansonga pa phiri, osiyidwa pamaso pa ana a Israyeli; ndipo padzakhala bwinja.

10 Cifukwa iwe waiwala Mulungu wa cipulumutso cako, sunakumbukira thanthwe la mphamvu zako; cifukwa cace iwe waoka mitengo yokondweretsa, waokapo zipinjiri zacilendo;

11 tsiku lako looka uzingapo mpanda, nuphukitsa mbeu zako m'mawa mwace; mulu wa masika udzaoneka tsiku lakulira ndi la cisoni cothetsa nzeru.

12 Ha, phokoso la mitundu yambiri ya anthu ambiri, amene apfuula ngati kukukuma kwa nyanja: ndi kuthamanga kwa amitundu, akuthamanga ngati kuthamangakwa madzi amphamvu!

13 Mitundu ya anthu idzathamanga ngati kuthamanga kwa madzi ambirimbiri; koma Iye adzawadzudzula, ndipo iwo adzathawira patari, nadzapitikitsidwa monga mankhusu a pamapiri patsogolo pa mphepo, ndi monga pfumbi lokwetera patsogolo pa mkunthu wa mphepo.

14 Pa nthawi ya madzulo, taonani kuopsya; kusanace, iwo palibe. Ili ndi gawo la iwo amene atifunkha ndi ici ciwagwera omwe alanda zathu.

18

1 Ha, dziko lakukupuza mapiko, liri tsidya lija la nyanja za Etiopia;

2 limene litumiza mithenga panyanja m'ngalawa zatnabungwa zoyenda m'madzi, ndi kuti, Mukani, inu mithenga yoyenda msanga msanga ku mtundu wa anthu atari ndi osalala, kwa mtundu woopsya cikhalire cao, mtundu umene uyesa dziko ndi kupondereza pansi, umene dziko lace nyanja ziligawa!

3 Inunonseakukhala m'dziko lapansi, ndi inu akukhazikika pa dziko lapansi, potukulidwa cizindikiro pamwamba pa mapiri, mudzaona, ndi polizidwa lipenga mudzamva.

4 Pakuti Yehova watero kwa ine, Ine ndidzakhala cete, ndipo ndidzayang'ana mokhala cete, ndipo ndidzayang'ana mokhalamo Ine, monga kuwala kotentha kwa dzuwa, monga mtambo wa mame m'kutentha kwa masika.

5 Pakuti masika asanafike, kutatha kuphuka ndi posanduka duwa mphesa yofuna kucha, iye adzadzombolera tinthambi ndi mphopo, ndi nthambi zotasa adzazicotsa ndi kuzisadza.

6 Adzasiyira mbalame zakulusa za m'mapiri ndi zirombo za dziko nthambizo, ndipo mbalame zakulusa zidzakhalapo m'dzinja, ndi zirombo zonse za dziko zidzakhalapo m'malimwe.

7 Nthawi imeneyo mphatso idzaperekedwa kwa Yehova wa makamu, mtundu wa anthu atari ndi osalala, yocokera kwa mtundu woopsya cikhalire cao; mtundu umene uyesa dziko ndi kupondereza pansi, umene dziko lace nyanja ziligawa, ku malo a dzina la Yehova wa makamu, phiri la Ziyoni.

19

1 Katundu wa Aigupto. Taonani, Yehova wakwera pamwamba pa mtambo wothamanga, nadza ku Aigupto; ndi mafano a Aigupto adzagwedezeka pakufika kwace, ndi mtima wa Aigupto udzasungunuka pakati pace.

2 Ndipo ndidzapikisanitsa Aaigupto; ndipo adzamenyana wina ndi mbale wace, ndi wina ndi mnansi wace; mudzi kumenyana ndi mudzi, ndi ufumu kumenyana ndi ufumu.

3 Ndipo mzimu wa Aigupto adzakhala wacabe pakati pace; ndipo Ine ndidzaononga uphungu wace; ndimo iwo adzafunafuna mafano ndi anyanga, ndi alauli, ndi obwebweta.

4 Ndipo ndidzapereka Aigupto m'manja mwa mbuye wankharwe; ndi mfumu yaukali idzawalamulira, ati Ambuye, Yehova wa makamu.

5 Ndipo madzi adzaphwa m'nyanja yaikuru, ndipo nyanja yoyendamo madzi idzaphwa, niuma.

6 Ndipo nyanja zidzanunkha; mitsinje ya Aigupto idzacepa, niuma; bango ndi mlulu zidzafota.

7 Madambo ovandikana ndi Nile, pafupi ndi gombe la Nile, ndi zonse zobzyala pa Nile zidzauma, nizicotsedwa, zosakhalanso konse.

8 Asodzinso adzalira, ndi onse oponya mbedza m'Nile adzaliralira, ndi onse oponya makoka m'madzi, adzalefuka.

9 Komanso iwo amene agwira nchito yakupala bwazi, ndi iwo amene aomba nsaru yoyera, adzakhala ndi manyazi.

10 Ndipo maziko ace adzasweka, onse amene agwira nchito yolipidwa adzabvutidwa mtima.

11 Akalonga a Zoani apusa ndithu; uphungu wa aphungu anzeru a Farao wasanduka wopulukira; bwanji iwe unena kwa Farao, Ine ndine mwana wa anzeru, mwana wa mafumu akale?

12 Nanga tsopano anzeru ali kuti? akuuze iwe tsopano; adziwe cimene Yehova wa makamu watsimikiza mtima kucitira Aigupto.

13 Akalonga a Zoani apusa, akalonga a Nofi anyengedwa; iwo asoceretsa Aigupto, amene ali mwala wa pangondya wa mapfuko ace.

14 Yehova wasanganiza mzimu wa kusaweruzika pakati pace; ndipo iwo asoceretsa Aigupto m'nchito zonse zace, monga mwamuna woledzera ayenda punzipunzi posanza pace.

15 Aigupto sadzakhala ndi nchito, imene mutu pena mcira, pena nthambi ya kanjedza, pena mlulu zidzaigwira.

16 Tsiku limenelo Aigupto adzanga akazi; ndipo adzanthunthumira ndi kuopa, cifukwa ca kugwedeza kwa dzanja la Yehova wa makamu, limene Iye agwedeza pamwamba pace.

17 Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa Aigupto, yense wakulichula adzamtembenukira mwamantha, cifukwa ca uphungu wa Yehova wa makamu, aupanga pa dzikolo.

18 Tsiku limenelo padzakhala midzi isanu m'dziko la Aigupto yolankhula cinenero ca Kanani, ndi yolumbira, Pali Yehova wa makamu; wina udzachedwa, Mudzi wa cionongeko.

19 Tsiku limenelo padzakhala guwa la nsembe la Yehova pakati pa dziko la Aigupto, ndi coimiritsa ca Yehova m'malire ace.

20 Ndipo cidzakhala cizindikiro ndi mboni ya Yehova wa makamu m'dziko la Aigupto; pakuti iwo adzalirira kwa Yehova, cifukwa ca osautsa, ndipo Iye adzawatumizira mpulumutsi, ndi wamphamvu, nadzawapulumutsa.

21 Ndipo Yehova adzadziwika kwa Aigupto, ndipo Aaigupto adzadziwa Yehova tsiku limenelo; inde iwo adzapembedzera ndi nsembe ndi zopereka, nadzawindira Yehova ndi kucitadi.

22 Ndipo Yehova adzakantha Aigupto kukantha ndi kuciritsa; ndipo iwo adzabwerera kwa Yehova, ndipo Iye adzapembedzedwa ndi iwo, nadzawaciritsa.

23 Tsiku limenelo padzakhala khwalala locokera m'Aigupto kunka ku Asuri, ndipo M-asuri adzafika ku Aigupto, ndi M-aigupto adzafika ku Asuri, ndipo Aaigupto adzapembedzera pamodzi ndi Aasuri.

24 Tsiku limenelo Israyeli ndi Aigupto ndi Asuri atatuwa, adzakhala mdalitso pakati pa dziko lapansi;

25 pakuti Yehova wa makamu wadalitsa iwo, ndi kuti, Odalitsika Aigupto anthu anga, ndi Asuri nchito ya manja anga, ndi Israyeli colowa canga.

20

1 Caka cimene kazembe wa ku Asuri anafika ku Asidodi, muja Sarigoni mfumu ya Asuri anamtumiza iye, ndipo iye anamenyana ndi Asidodi, naugonjetsa.

2 Nthawi imeneyo Yehova ananena ndi Yesaya, mwana wa Amozi, nati, Muka numasule ciguduli m'cuuno mwako, nucicotse, nubvule nsapato yako ku phazi lako. Ndipo iye anatero, nayenda marisece, ndi wopanda nsapato,

3 Ndipo Yehova anati, Monga mtumiki wanga Yesaya wayenda marisece ndi wopanda nsapato zaka zitatu, akhale cizindikilo ndi codabwitsa kwa Aigupto ndi kwa Etiopia;

4 momwemo mfumu ya Asuri idzatsogolera kwina am'nsinga a Aigupto, ndi opitikitsidwa a Etiopia, ana ndi okalamba, amarisece ndi opanda nsapato, ndi matako osabvala, kuti acititse manyazi Aigupto.

5 Ndipo iwo adzakhala ndi mantha ndi manyazi, cifukwa ca Kusi, amene anawatama, ndi Aigupto, amene anawanyadira.

6 Ndipo wokhala m'mphepete mwa nyanja muno adzati tsiku limenelo, Taonani, kuyembekeza kwathu kuli kotero, kumene ife tinathawira atithangate kupulumutsidwa kwa mfumu ya Asuri, ndipo ife tidzapulumuka bwanji?

21

1 Katundu wa cipululu ca kunyanja. Monga akabvumvulu a kumwela apitirira, kufumira kucipululu ku dziko loopsya.

2 Masomphenya obvuta aonetsedwa kwa ine; wogula malonda wonyenga amangonyenga, ndi wofunkha amangofunkha. Kwera Elamu iwe; zunguniza Media iwe; kuusa moyo kwace konse ndakutonthoza.

3 Cifukwa cace m'cuuno mwanga mwadzazidwa ndi zopota; zopweteka zandigwira ine monga zopweteka za mkazi pobala mwana; zowawa zindiweramitsa, makutu anga sangathe kumva; ndicita mantha sindingathe kuona.

4 Mtima wanga uguguda, mantha andiopsetsa ine; cizitezite cimene ndinacikhumba candisandukira kunthunthumira.

5 Iwo akonza pa gome lodyera, aika alonda, adya, namwa; ukani, akalonga inu, dzozani mafuta cikopa.

6 Pakuti Ambuye atero kwa ine, Muka, ika mlonda anene cimene aciona;

7 ndipo pamene iye anaona khamu, amuna apakavalo awiri awiri, khamu la aburu, khamu la ngamila, iye adzamvetsera ndi khama mosamalitsa.

8 Ndipo iye anapfuulitsa ngati mkango, Ambuye inu, ine ndiimabe pamwamba pa nsanja nthawi ya usana, ndipo ndiikidwa mu ulonda wanga usiku wonse;

9 ndipo taonani, kuno kulinkudza khamu la amuna, apaakavalo awiri awiri. Ndipo iye anayankha nati, Babulo wagwa, wagwa; ndi mafano onse osema a milungu yace asweka, nagwa pansi.

10 Kuomba kwanga nanga, ndi za pa dwale langa: cimene ine ndinacimva kwa Yehova wa makamu Mulungu wa Israyeli, ndanena kwa inu.

11 Katundu wa Duma. Wina aitana kwa ine kucokera ku Seiri, Mlonda, nthawi yanji ya usiku? Mlonda, nthawi yanji ya usiku?

12 Mlonda anati, Kuli kuca, koma kukali usiku; mukafuna kufunsa, funsani, bwerani, idzani.

13 Katundu wa pa Arabiya. M'nkhalango ya m'Arabiya mudzagona, inu makamu oyendayenda a Dedani.

14 Mucingamire akumva ludzu ndi madzi; okhala m'dziko la Tema ananka kukomana ndi othawa ndi cakudya cao.

15 Pakuti iwo anathawa malupanga, malupanga osololedwa, ndi mauta-olifuka ndi nkhondo yobvuta.

16 Pakuti Ambuye ana tero kwa ine, Cisanapite caka malinga ndi zaka za wolembedwa nchito ulemerero wonse wa Kedara udzagoma;

17 ndi otsala amauta, ngwazi za ana a Kedara zidzacepa, pakuti Yehova Mulungu wa Israyeli wanena.

22

1 Katundu wa cigwa ca masomphenya. Mwatani kuti mwakwera nonsenu pamacindwi?

2 Iwe amene wadzala ndi zimpfuu, mudzi waphokoso, mudzi wokondwa; ophedwa ako, sanaphedwa ndi lupanga, sanafe m'nkhondo.

3 Olamulira ako onse athawa pamodzi, anamangidwa ndi amauta; opezedwa ako onse anamangidwa pamodzi, nathawira patari.

4 Comweco ndinati, Usandiyang'ane ine, ndilira ndi kuwawa mtima; usafulumire kunditonthoza ine, cifukwa ca kufunkhidwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga,

5 Pakuti ndi tsiku laphokoso, ndi lopondereza pansi, ndi lothetsa nzeru, locokera kwa Ambuye Yehova wa makamu, m'cigwa ca masomphenya, kugumuka kwa malinga, ndi kupfuulira kumapiri.

6 Ndipo Elamu anatenga phodo, ndi magareta a anthu ndi apakavalo; ndipo Kiri anaonetsa zikopa.

7 Ndipo panali kuti zigwa zako zosankhika zinadzala magareta, ndi apakavalo anadzinika okha pacipata.

8 Ndipo Iye anacotsa cophimba ca Yuda; ndipo iwe unayang'ana tsiku limenelo pa zida za m'nyumba ya nkhalango.

9 Ndipo inu munaona kuti pa mudzi wa Davide panagumuka mipata yambiri; ndipo munasonkhanitsa pamodzi madzi a m'thamanda lakunsi.

10 Ndipo inu munawerenga nyumba za Yerusalemu, ndipo munagwetsa nyumba, kuti mumangire linga.

11 Inu munapanganso cosungamo madzi a thamanda lakale, pakati pa malinga awiri; koma inu simunamuyang'ane iye amene anacicita ico, ngakhale kusamalira iye amene analipanga kale.

12 Ndipo tsiku limenelo Ambuye, Yehova wa makamu, anaitana kulira, ndi kugwa misozi, ndi kumeta, ndi kubvala ciguduli m'cuuno;

13 koma taonani, kukondwa, ndi kusekerera, ndi kupha ng'ombe, ndi kupha nkhosa, ndi kudya nyama, ndi kumwa vinyo; tiyeni tidye ndi kumwa, cifukwa mawa tidzafa.

14 Ndipo Yehova wa makamu wadzibvumbulutsa yekha m'makutu mwanga, Ndithu coipa cimeneci sicidzacotsedwa pa inu kufikira inu mudzafa, ati Ambuye, Yehova wa makamu.

15 Atero Ambuye Yehova wa makamu, Muka, pita iwe kwa kapitao uyu, kwa Sebina woyang'anira nyumba, ndi kuti,

16 Ucitanji iwe kuno, ndimo ndani ali nawe kuno, kuti iwe wagoba manda kuno, ndi kudzigobera manda pamwamba, ndi kudzisemera mogonamo m'thanthwe.

17 Taona Yehova adzakuponya iwe zolimba, monga mwamuna wamphamvu, inde adzakufumbata zolimba.

18 Iye ndithu adzakuzunguza, ndi kukuponyaponya ngati mpira m'dzido lalikuru; kumeneko iwe udzafa, ndipo kumeneko kudzakhala magareta a ulemerero wako, iwe wocititsa manyazi banja la mbuye wako.

19 Ndipo Ine ndidzakuturutsa iwe mu nchito yako, ndi kukutsitsa iwe pokhala pako.

20 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti ine ndidzaitana mtumiki wanga, Eliakimu mwana wa Hilikiya:

21 ndipo ndidzambveka iye cobvala cako, ndi kumlimbikitsa ndi lamba lako, ndipo ndidzapereka ulamuliro wako m'dzanja lace; ndipo iye adzakhala atate wa okhala m'Yerusalemu ndi a nyumba ya Yuda.

22 Ndipo ndidzaika mfungulo wa nyumba ya Davide paphewa pace, ndipo iye adzatsegula, ndipo palibe wina adzatseka, iye adzatseka ndipo palibe wina adzatsegula.

23 Ndipo ndidzamkhomera iye ngati msomali polimba; ndipo iye adzakhala mpando wa ulemerero wa banja la atate wace.

24 Ndipo iwo adzapacika pa iye ulemerero wonse wa banja la atate wace, obadwa ndi ana, mbiya zonse zazing'ono, ngakhale zikho ndi aguda omwe.

25 Tsiku limenelo, ati Yehova wa makamu, msomali wokhomeredwa polimba udzasukusika; nudzaguluka, ndi kugwa, ndi katundu wopacikidwapo adzadulidwa; pakuti Yehova wanena.

23

1 Katundu wa Turo. Kuwani, inu ngalawa za Tarisi; cifukwa wapasudwa, kulibenso nyumba, kulibe polowera; kucokera ku dziko la Kitimo kwabvumbulutsidwa kwa iwo.

2 Khalani cete, inu okhala m'cisumbu; iwe amene anakudzazanso amalonda a ku Zidoni, opita m'nyanja.

3 Ndi pa nyanja zazikuru anapindula ndi mbeu za ku Sihori ndizo dzinthu za ku Nile; ndi kumeneko kunali msika wa amitundu.

4 Khala ndi manyazi, iwe Zidoni; cifukwa nyanja yanena, linga la kunyanja, ndi kuti, Ine sindinamve zowawa, kapena kubala, kapena kulera anyamata, kapena kulera anamwali.

5 Pofika mbiriyo ku Aigupto, iwo adzamva kuwawa kwambiri pa mbiri ya Turo.

6 Olokani inu, kunka ku Tarisi, kuwani, inu okhala m'cisumbu.

7 Kodi umene ndi mudzi wanu wokondwa, wacikhalire kale lomwe, umene mapazi ace anaunyamula kunka nao kutari kukhalako?

8 Ndani wapanga uphungu uno pa Turo, mudzi umene upereka akorona, amalonda ace ali akalonga, ogulitsa ace ali olemekezeka pa dziko lapansi?

9 Yehova wa makamu wapanga uphungu uwu, kuipitsa kunyada kwa ulemerero wonse, kupepula onse olemekezeka a m'dziko lapansi.

10 Pita pakati pa dziko lako monga Nile, iwe mwana wamkazi wa Tarisi; palibenso lamba.

11 Iye watambasula dzanja lace panyanja, wagwedeza maufumu; Yehova walamulira za amalonda, kupasula malinga ace.

12 Ndipo Iye anati, Iwe sudzakondwanso konse, iwe namwali wobvutidwa, mwanawamkazi wa Zidoni; uka, oloka kunka ku Kitimu; ngakhale kumeneko iwe sudzapumai.

13 Taonani, dziko la Akasidi; anthu awa sakhalanso; Asuri analiika ilo likhale la iwo okhala m'cipululu; iwo amanga nsanja zao, nagumula nyumba za mafumu ace; nalipasula.

14 Kuwani, inu ngalawa za Tarisi; pakuti linga lanu lapasulidwa.

15 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti Turo adzaiwalika zaka makumi asanu ndi awiri, malinga ndi masiku a mfumu imodzi; zitapita zaka makumi asanu ndi ziwirizo, cidzakhala kwa Turo monga m'nyimbo ya mkazi wadama.

16 Tenga mngoli, yendayenda m'mudzi, iwe mkazi wadama, amene unaiwalika; yimba zokoma, curukitsa nyimbo, kuti ukumbukiridwe.

17 Ndipo padzali, zitapita zaka makumi asanu ndi awirizo, kuti Yehova adzazonda Turo, ndipo iye adzabwerera ku mphotho yace, nadzacita dama ndi maufumu onse a dziko lapansi, okhala kunja kuno.

18 Malonda ace ndi mphotho yace zidzakhala zopatulikira Yehova; sizidzasungidwa kapena kuikidwa; cifukwa malonda ace adzakhala kwa iwo, amene akhala pamaso pa Yehova, kuti adye mokwana, nabvale caulemu.

24

1 Taonani, Yehova apululutsa dziko, nalipasula, nalitembenuza dodolido, nabalalitsa okhalamo ace.

2 Ndipo padzakhala monga ndi anthu, moteronso ndi ansembe; monga ndi mtumiki, moteronso ndi mbuyace; monga ndi mdzakazi, moteronso ndi mbuyace wamkazi; monga ndi wogula, moteronso ndi wogulitsa; monga ndi wobwereka, moteronso ndi wombwereka; monga ndi wotenga phindu, moteronso ndi wombwezera phindu kwa iye.

3 Dziko lidzapululuka konse, ndi kupasulidwa ndithu; pakuti Yehova ananena mau amenewa.

4 Dziko lilira nilifota, dziko lilefuka nilifota, anthu omveka a padziko alefuka.

5 Dzikonso laipitsidwa ndi okhalamo ace omwe, cifukwa iwo alakwa pamalamulo nasinthanitsa malemba, natyola cipangano ca nthawi zonse.

6 Cifukwa cace citemberero cadya dziko, ndi amene akhala m'menemo apezedwa ocimwa, cifukwa cace okhalamo a padziko atenthedwa, ndipo anthu owerengeka atsala.

7 Vinyo watsopano alira, mpesa ulefuka, mitima yonse yokondwa iusa moyo.

8 Kusangalala kwa mangaka kwalekeka, phokoso la iwo amene aserera litha, kukondwa kwa mngoli kwalekeka.

9 Iwo sadzamwa vinyo ndi kuyimba nyimbo; cakumwa caukali cidzawawa kwa iwo amene acimwa.

10 Mudzi wosokonezeka wagwetsedwa pansi; nyumba zonse zatsekedwa, kuti asalowemo munthu.

11 Muli mpfuu m'makwalala cifukwa ca vinyo; kukondwa konse kwadetsedwa, kusangalala kwa dziko kwatha.

12 M'mudzi mwatsala bwinja, ndi cipata camenyedwa ndi cipasuko.

13 Cifukwa cace padzakhala cotero pakati pa dziko mwa anthu, ngati kugwedeza kwa mtengo waazitona, ngati khunkha la mphesa, pakutha masika ace.

14 Amenewa adzakweza mau ao, nadzapfuula; cifukwa ca cifumu ca Yehova, iwo adzapfuula zolimba panyanja.

15 Cifukwa cace lemekezani inu Yehova kum'mawa, ngakhale dzina la Yehova, Mulungu wa Israyeli, m'zisumbu za m'nyanja.

16 Kucokera ku malekezero a dziko ife tamva nyimbo zolemekeza wolungama. Koma ine ndinati, Ndaonda ine, ndaonda ine, tsoka kwa ine! amalonda onyenga amangonyenga; inde ogulitsa onyenga apambana kunyenga.

17 Mantha ndi dzenje ndi msampha ziri pa iwe, wokhala m'dziko.

18 Ndipo padzali, kuti iye amene athawa mbiri yoopsya, adzagwa m'dzenje; ndi iye amene aturuka m'kati mwa dzenje, adzakodwa mumsampha, pakuti mazenera a kuthambo atsegudwa, ndi maziko a dziko agwedezeka.

19 Dziko lapansi lasweka ndithu, dziko lapansi lasungunukadi, dziko lapansi liri kugwedezeka kopambana.

20 Dziko lapansi lidzacita dzandi dzandi, ngati munthu woledzera, ndi kunjenjemera, ngati cilindo; ndi kulakwa kwace kudzalilemera, ndipo lidzagwa losaukanso.

21 Ndipo padzali tsiku limenelo, kuti Yehova adzazonda kumwamba khamu la kumwamba, ndi mafumu a dziko lapansi.

22 Ndipo iwo adzasonkhanitsidwa pamodzi, monga ndende zimasonkhanitsidwa m'dzenje, ndi kutsekeredwa m'kaidi, ndipo atapita masiku ambiri adzawazonda.

23 Pompo mwezi udzanyazitsidwa, ndi dzuwa lidzakhala ndi manyazi, pakuti Yehova wa makamu adzalamulira caulemerero m'phiri la Ziyoni, ndi m'Yerusalemu, ndi pamaso pa akuru akuru ace.

25

1 Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga, ndidzakukuzani Inu, ndidzatamanda dzina lanu, cifukwa mwacita zinthu zodabwitsa, ngakhale: zauphungu zakale, mokhulupirika ndi m'zoonadi.

2 Cifukwa Inu mwasandutsa mudzi muunda; mudzi walinga bwinja; nyumba ya alendo kuti isakhale mudzi; sudzamangidwa konse.

3 Cifukwa cace anthu amphamvu adzakulemekezani Inu, mudzi wa mitundu yakuopsya udzakuopani Inu.

4 Cifukwa Inu mwakhala linga la aumphawi, linga la osowa m'kubvutidwa kwace, pobisalira cimphepo, mthunzi wa pa dzuwa, pamene kuomba kwa akuopsya kufanana ndi cimphepo cakuomba chemba.

5 Monga kutentha m'malo ouma, Inu mudzaletsa phokoso la alendo; nyimbo ya akuopsya idzaletseka, monga mthunzi uletsa dzuwa.

6 Ndipo m'phiri limendi Yehova wa makamu adzakonzera anthu ace onse phwando la zinthu zonona, phwando la vinyo wa pamitsokwe, la zinthu zonona za mafuta okha okha, la vinyo wansenga wokuntha bwino.

7 Ndipo Iye adzaononga m'phiri limeneli cophimba nkhope cobvundikira mitundu yonse ya anthu, ndi nsaru yokuta amitundu onse.

8 Iye wameza imfa ku nthawi yonse; ndipo Ambuye Mulungu adzapukuta misozi pa nkhope zonse; ndipo citonzo ca anthu ace adzacicotsa pa dziko lonse lapansi; cifukwa Yehova wanena.

9 Ndipo adzanena tsiku limenelo, Taonani, uyu ndiye Mulungu wathu; tamlindirira Iye, adzatipulumutsa; uyu ndiye Yehova, tamlindirira Iye, tidzakondwa ndikusekereram'cipulumutso cace.

10 Cifukwa m'phiri limeneli dzanja la Yehova lidzakhalamo, ndipo Moabu adzaponderezedwa pansi m'malo ace, monga maudzu aponderezedwa padzala.

11 Ndipo iye adzatambasula manja ace pakati pamenepo, monga wosambira atambasula manja ace posambira; koma Iye adzagwetsa pansi kunyada kwace, pamodzi ndi kunyenga kwa manja ace.

12 Ndipo linga la pamsanje la macemba ako Iye waligwetsa, naligonetsa pansi, nalifikitsa padothi, ngakhale papfumbi.

26

1 Tsiku limenelo adzayimba nyimbo imeneyi m'dziko la Yuda, Ife tiri ndi mudzi wolimba; Iye adzaikacipulumutso cikhale macemba ndi malinga.

2 Tsegulani pazipata, kuti mtundu wolungama, umene ucita zoonadi, ulowemo.

3 Inu mudzasunga mtima wokhazikika mu mtendere weni weni, cifukwa ukukhulupirirani Inu.

4 Khulupirirani Yehova nthawi zamuyaya, pakuti mwa Ambuye Yehova muli thanthwe lacikhalire.

5 Cifukwa Iye watsitsira pansi iwo amene anakhala pamwamba, mudzi wa pamsanje; Iye wautsitsa, wautsitsira pansi; waugwetsa pansi pa pfumbi.

6 Phazi lidzaupondereza pansi; ngakhale mapazi a aumphawi, ndi mapondedwe a osowa.

7 Njira ya wolungama iri njira yoongoka; Inu amene muli woongoka, mukonza njira ya wolungama.

8 Inde m'njira ya maweruziro anu, Yehova, ife talindira Inu; moyo wathu ukhumba dzina lanu, ndi cikumbukilo canu.

9 Ndi moyo wanga ndinakhumba Inu usiku; inde ndi mzimu wanga wa mwa ine ndidzafuna Inu mwakhama; pakuti pamene maweruziro anu ali pa dziko lapansi, okhala m'dziko lapansi adzaphunzira cilungamo.

10 Ungayanje woipa, koma sadzaphunzira cilungamo; m'dziko la macitidwe oongoka, iye adzangocimwa, sadzaona cifumu ca Yehova.

11 Yehova, dzanja lanu litukulidwa, koma iwo saona; koma iwo adzaona cangu canu ca kwa anthu, nadzakhala ndi manyazi; inde moto udzamariza adani anu.

12 Yehova, udzatikhazikitsira mtendere; pakuti mwatigwirira nchito zathu zonse.

13 Yehova Mulungu wathu, pamodzi ndi Inu ambuye ena adatilamulira ife; koma mwa Inu nokha tidzachula dzina lanu.

14 Iwo afa, atha, sadzakhalanso ndi moyo; ali mizimu, sadzauka; cifukwa cace Inu munawazonda, ndi kuwaononga, mwathetsa cikumbukiro cao conse.

15 Mwacurukitsa mtundu, Yehova, mwacurukitsa mtundu; Inu mwalemekezeka, mwakuza malire onse a dziko.

16 Yehova, iwo adza kwa Inu mobvutika, iwo anathira pemphero, muja munalikuwalanga.

17 Monga ngati mkazi wokhala ndi pakati, amene nthawi yace yakubala yayandikira, amva zopweteka, ndi kupfuula m'zowawa zace; momwemo takhala ife pamaso panu, Yehova.

18 Ife tinali ndi pakati, ife tinamva zopweteka, tafanana ngati tabala mphepo; sitinacite cipulumutso ciri conse pa dziko lapansi; ngakhale okhala m'dziko lapansi sanagwe.

19 Akufa anu adzakhala ndi moyo; mitembo yao idzauka. Ukani muyimbe, inu amene mukhala m'pfumbi; cifukwa mame ako akunga mame a pamasamba, ndipo dziko lapansi lidzaturutsa mizimu.

20 Idzani, anthu anga, lowani m'zipinda mwanu, nimutseke pamakomo panu; nimubisale kanthawi kufikira mkwiyo utapita.

21 Pakuti taonani, Yehova adza kucokera ku malo ace kudzazonda okhala pa dziko lapansi, cifukwa ca kuipa kwao; dziko lidzabvumbulutsa mwazi wace, ndipo silidzabvundikiranso ophedwa ace.

27

1 Tsiku limenelo Yehova ndi lupanga lace lolimba ndi lalikuru ndi lamphamvu adzalanga nangumi njoka yotamanga, ndi nangumi njoka yopindika-pindika; nadzapha cing'ona cimene ciri m'nyanja.

2 Tsiku limenelo: munda wa mphesa wavinyo, yimbani inu za uwo.

3 Ine Yehova ndiusunga uwo; ndidzauthirira madzi nthawi zonse; ndidzausunga usiku ndi usana, kuti angauipse.

4 Ndiribe ukali; ndani adzalimbanitsa lunguzi ndi minga ndi Ine kunkhondo? ndiziponde ndizitenthe pamodzi.

5 Kapena mlekeni, agwire mphamvu zanga, nacite nane mtendere; inde, acite nane mtendere.

6 M'mibadwo ikudzayo Yakobo adzamera mizu; Israyeli adzaphuka ndi kucita mphundu; ndipo iwo adzadzaza ndi zipatso pa dziko lonse lapansi.

7 Kodi Mulungu wakantha Yakobo, monga umo anawakanthira akumkanthawo? kapena kodi iye waphedwa malinga ndi kuphedwa kwa iwo amene anaphedwa ndi iye?

8 Munalimbana naye pang'ono, pamene munamcotsa; wamcotsa iye kuomba kwace kolimba tsiku la mphepo yamlumbanyanja.

9 Cifukwa cace, mwa ici coipa ca Yakobo cidzafafanizidwa, ndipo ici ndi cipatso conse cakucotsa cimo lace; pamene iye adzayesa miyala yonse ya guwa la nsembe, ngati miyala yanjeresa yoswekasweka, zifanizo ndi mafano a dzuwa sizidzaukanso konse.

10 Pakuti mudzi wocingidwa uli pa wokha, mokhalamo mwa bwinja, ndi mosiyidwa ngati cipululu; mwana wa ng'ombe adzadya kumeneko, nadzagonako pansi, nadzamariza nthambi zace.

11 Ponyala nthambi zace zidzatyoledwa; akazi adzafika, nazitentha ndi moto, pakuti ali anthu opanda nzeru; cifukwa cace Iye amene anawalenga sadzawacitira cisoni, ndi Iye amene anawaumba sadzawakomera mtima.

12 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti Yehova adzaomba tirigu wace, kucokera madzi a nyanja, kufikira ku mtsinje wa Aigupto, ndipo mudzakunkhidwa mmodzi, inu ana a Israyeli.

13 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, lipenga lalikuru lidzaombedwa; ndipo adzafika omwe akadatayika m'dziko la Asuri, ndi opitikitsidwa a m'dziko la Aigupto; ndipo adzapembedza Yehova m'phiri lopatulika la pa Yerusalemu.

28

1 Tsoka kwa korona wakunyada wa oledzera a Efraimu, ndi kwa duwa lakufota la ulemerero wace wokongola, limene liri pamutu paiwo, amene agwidwa ndi vinyo, m'cigwa ca nthaka yabwino.

2 Taonani, Ambuye ali ndi wina wamphamvu wolimba; ngati cimphepo ca matalala, mkuntho wakuononga, ngati namondwe wa madzi amphamvu osefukira, adzagwetsa pansi ndi dzanja lamphamvu.

3 Korona wakunyada wa oledzera a Efraimu adzaponderezedwa;

4 ndi duwa lakufota la ulemerero wace wokongola, limene liri pamutu pa cigwa ca nthaka yabwino, lidzakhala ngati nkhuyu yoyamba kuca malimwe asanafike; polona wakupenya imeneyo, amaidya iri m'dzanja lace.

5 Tsiku limenelo Yehova wa makamu adzakhala korona wa ulemerero, ndi korona wokongola kwa anthu ace otsala:

6 ndipo adzakhala mzimu wa ciweruziro kwa oweruza mirandu, ndi mphamvu kwa iwo amene abweza nkhondo pacipata.

7 Koma iwonso adzandima ndi vinyo, nasocera ndi cakumwa caukali, wansembe ndi mneneri adzandima ndi cakumwa caukali, iwo amezedwa ndi vinyo, nasocera ndi cakumwa caukali, adzandima popenya, napunthwa poweruza.

8 Pakuti magome onse adzazidwa ndi masanzi ndi udio, palibe malo okonzeka.

9 Kodi Mulungu adzaphunzitsa yani nzeru? Kodi Iye adzamvetsa yani uthengawo? iwo amene aletsedwa kuyamwa, nacotsedwa pamabere?

10 Pakuti pali langizo ndi langizo, langizo ndi langizo; lamulo ndi lamulo, lamulo ndi lamulo; kuno pang'ono, uko pang'ono.

11 Iai, koma ndi anthu a milomo yacilendo, ndi a lilume lina, Iye adzalankhula kwa anthu awa;

12 amene ananena nao, Uku ndi kupuma, mupumitsa wolema, ndi apa ndi potsitsimutsa, koma iwo anakana kumva.

13 Cifukwa cace mau a Yehova adzakhala kwa iwo langizo ndi langizo, langizo ndi langizo; lamulo ndi lamulo, lamulo ndi lamulo; kuno pang'ono, uko pang'ono; kuti ayende ndi kugwa cambuyo, ndi kutyoka, ndi kukodwa mumsampha, ndi kugwidwa.

14 Cifukwa cace imvani mau a Yehova, inu amuna amnyozo, olamulira anthu awa a m'Yerusalemu.

15 Cifukwa inu munati, Ife tapangana pangano ndi imfa, tabvomerezana ndi kunsi kwa manda; pakuti mliri wosefukira sudzatifikira ife; pakuti tayesa mabodza pothawirapo pathu, ndi kubisala m'zonyenga;

16 cifukwa cace Ambuye Yehova atero, Taonani, ndiika m'Ziyoni mwala wa maziko, mwala woyesedwa mwala wa pangondya, wa mtengo wace wokhazikika ndithu; wokhulupirira sadzafulumira.

17 Ndipo ndidzayesa ciweruziro cingwe coongolera, ndi cilungamo cingwe colungamitsira ciriri; ndipo matalala adzacotsa pothawirapo mabodza, ndi madzi adzasefukira mobisalamo.

18 Ndipo pangano lanu ndi imfa lidzathedwa, ndi kubvomerezana kwanu ndi kunsi kwa manda kudzalepereka; popita mliri woopsya udzakuponderezani pansi.

19 Nthawi zonse umapita, udzakutengani; cifukwa m'mawa ndi m'mawa udzapita, usana ndi usiku; ndipo kudzakhala kuopsya kokha, kumva mbiri yace.

20 Pakuti kama wafupika, munthu sangatambalale pamenepo; ndi copfunda cacepa, sicingamfikire.

21 Pakuti Yehova adzauka monga m'phiri la Perazimu, nadzakwiya monga m'cigwa ca Gibeoni; kuti agwire nchito yace, nchito yace yacilendo, ndi kuti acite cocita cace, cocita cace cacilendo.

22 Tsono musakhale amnyozo, kuti nsinga zanu zingalimbe; pakuti Ambuye, Yehova wa makamu, wandimvetsa za cionongeko cotsimikizidwa pa dziko lonse lapansi.

23 Cherani inu makutu, imvani mau anga; mverani, imvani kulankhula kwanga.

24 Kodi mlimi amalimabe kuti abzale? kodi amacocolabe, ndi kuswa zibuma za nthaka?

25 Atakonza tyatyatya pamwamba pace, kodi safesa ponse mawere, ndi kumwazamwaza citowe, nafesa tirigu m'mizere ndi barele m'malo ace osankhika, ndi mcewere m'maliremo?

26 Pakuti Mulungu wace amlangiza bwino namphunzitsa.

27 Pakuti sapuntha mawere ndi copunthira cakuthwa, ngakhale kuzunguniza njinga ya gareta pacitowe; koma amakulunga mawere ndi munsi, naomba citowe ndi cibonga.

28 Tirigu wa mkate aperedwa; pakuti samampuntha osaleka; ngakhale kuyendetsapo njinga ya gareta wace, ngakhale kumphwanya ndi ziboda za akavalo ace sapera.

29 Icinso cifumira kwa Yehova wa makamu, uphungu wace uzizwitsa ndi nzeru yace impambana.

29

1 Eya Arieli, Arieli, mudzi umene Davide anamangapo zithando! oniezerani caka ndi caka; maphwando afikenso;

2 pamenepo ndidzasautsa Arieli, ndipo padzakhala maliro ndi kulira; koma iye adzakhala kwa Ine monga Arieli.

3 Ndipo ndidzamanga zithando kuzungulira iwe ponse, ndipo ndidzamanga linga ndi kuunjika miulu yakumenyanirana ndi iwe.

4 Ndipo iwe udzagwetsedwa pansi, nudzanena uli pansi, ndi kulankhula kwako kudzakhala pansi koturuka m'pfumbi; ndi mau ako adzakhala ngati a wina amene ali ndi mzimu wobwebweta, kucokera pansi, ndi kulankhula kwako kudzakhala konong'ona kocokera m'pfumbi,

5 Koma khamu la acilendo ako lidzafanana ndi pfumbi losalala, ndi khamu la oopsya lidzakhala monga mungu wocokacoka; inde kudzaoneka modzidzimuka dzidzidzi.

6 Ndipo Yehova wa makamu adzamzonda ndi bingu, ndi cibvomezi, ndi mkokomo waukuru, kabvumvulu, ndi mkuntho, ndi lawi la moto wonyambita.

7 Ndipo khamu la mitundu yonse yomenyana ndi Arieli, ngakhale yonse yomenyana naye ndi linga lace, ndi kumsautsa idzafanana ndi loto, masomphenya a usiku.

8 Ndipo kudzafanana ndi munthu wanjala, pamene alota, ndipo, taonani, akudya; koma auka, ndipo m'kati mwace muli zi; kapena monga munthu waludzu pamene alota, ndipo, taonani, akumwa; koma auka ndipo taonani walefuka, ndipo m'kati mwace muli gwa; momwemo lidzakhala khamu la mitundu yonse yomenyana ndi phiri la Ziyoni.

9 Khalani ndi kudabwa; sangalalani ndi kukhala akhungu; iwo aledzera, koma si ndi vinyo, ali dzandi dzandi; koma si ndi cakumwa caukali.

10 Pakuti Yehova watsanulira pa inu mzimu wa tulo togonetsa, natseka maso anu, ndiwo aneneri; naphimba mitu yanu, ndiwo alauli.

11 Ndipo masomphenya onse akusandukirani mau a m'buku limatidwa ndi phula, limene anthu amapereka kwa wina wodziwa kuwerenga, nati, Werengani umu; koma ati, Sindingathe, cifukwa lamatidwa ndi phula;

12 ndipo buku laperekedwa kwa wosadziwa kuwerenga, ndi kuti, Werengani umu; koma ati, Ine sindinaphunzira.

13 Ndipo Ambuye anati, Popeza anthu awa ayandikira ndi Ine ndi m'kamwa mwao, nandilemekeza ndi milomo yao, koma mtima wao uli kutari ndi Ine, ndi mantha ao akundiopa Ine, ndi lamulo la anthu analiphunzira;

14 cifukwa cace, taonani, ndidzacitanso mwa anthu awa nchito yodabwitsa, ngakhale nchito yodabwitsa ndi yozizwitsa; ndipo nzeru ya anthu ao anzeru idzatha, ndi luntha la anthu ao ozindikira lidzabisika.

15 Tsoka kwa iwo amene afunitsa kubisira Yehova uphungu wao, ndi nchito zao ziri mumdima, ndipo amati Ndani ationa ife? ndani atidziwa ife?

16 Ozolitsa inu! Kodi woumba adzayesedwa ngati dothi; kodi cinthu copangidwa cinganene za iye amene anacipanga, Iye sanandipanga ine konse; kapena kodi cinthu coumbidwa cinganene za iye amene anaciumba, Iye alibe nzeru?

17 Kodi sikatsala kamphindi kakang'ono, ndipo Lebano adzasanduka munda wobalitsa, ndi munda wobalitsa udzayesedwa nkhalango?

18 Ndipo tsiku limenelo gonthi adzam va mau a m'buku, ndi maso akhungu adzaona poturuka m'zoziya ndi mumdima.

19 Ofatsanso kukondwa kwao kudzacuruka mwa Yehova, ndi aumphawi a mwa anthu adzakondwerera mwa Woyera wa Israyeli.

20 Pakuti woopsya wagoma, ndi wonyoza watha, ndi onse odikira zolakwa alikhidwa;

21 amene apalamulitsa munthu mlandu, namchera msampha iye amene adzudzula pacipata, nambweza wolungama ndi cinthu cacabe.

22 Cifukwa cace Yehova amene anaombola Abrahamu, atero za banja la Yakobo: Yakobo sadzakhala ndi manyazi tsopano, ngakhale nkhope yace tsopano sidzagwa.

23 Koma pamene iye aona ana ace, nchito ya manja anga, pakati pa iye, iwo adzayeretsa dzina langa; inde, iwo adzayeretsa Woyera wa Yakobo, nadzaopa Mulungu wa Israyeli.

24 Iwonso osocera mumzimu adzadziwa luntha, ndi iwo amene ang'ung'udza adzaphunzitsidwa.

30

1 Tsoka okhulupirira Aigupto. Tsoka kwa ana opanduka, ati Yehova, amene atenga uphungu koma si pa Ine; napangana pangano opanda mzimu wanga, kuti aonjezere cimo ndi cimo;

2 amene ayenda kutsikira ku Aigupto, osafunsa kukamwa kwanga, kudzilimbitsa iwo okha ndi li mphamvu za Farao, ndi kukhulupirira mthunzi wa Aigupto

3 Cifukwa cace mphamvu za Farao zidzakhala kwa inu manyazi, ndi kukhulupirira mthunzi wa Aigupto kudzakhala cisokonezo canu.

4 Pakuti akalonga ace ali pa Zaani, ndi mithenga yace yafika ku Hanesi.

5 Iwo onse adzakhala ndi manyazi, ndi anthu amene sangapindule nao kanthu, amene sakhala kwa iwo thangata, pena phindu, koma manyazi ndi citonzo.

6 Katundu wa zirombo za kumwera. M'dziko lobvuta ndi lopweteka, kumeneko kucokera mkango waukazi, ndi wamphongo, mphiri, ndi njoka youluka yamoto, iwo anyamula cuma cao pamsana pa aburu, ndi ang'ono zolemera zao pa malinundu a ngamila, kunka kwa anthu amene sadzapindula nao.

7 Pakuti thangata la Aigupto liri lacabe, lopanda pace; cifukwa cace ndamucha wonyada, wokhala cabe.

8 Tsopano pita, ukalembe mauwa pamaso pao pathabwa, nuwalembe m'buku, kuti akakhalebe ku nthawi yam'tsogolo, mboni ya masiku onse.

9 Pakuti ali anthu opanduka, ana onama, ana osafuna kumva cilamulo ca Yehova;

10 amene amati kwa alauli, Mtima wanu usapenye; ndi kwa aneneri, Musanenere kwa ife zinthu zoona, munene kwa ife zinthu zamyadi, munenere zonyenga;

11 cokani inu munjira, patukani m'bande, tiletsereni Woyera wa Israyeli pamaso pathu.

12 Cifukwa cace atero Woyera wa Israyeli, Popeza inu mwanyoza mau awa, nimukhulupirira nsautso ndi mphulupulu, ndi kukhala m'menemo;

13 cifukwa cace kuipa kumeneku kudzakhala kwa inu monga pogumuka pofuna kugwa, monga potukuka m'khoma lalitari, kugumuka kwace kufika modzidzimutsa dzidzidzi.

14 Ndipo Iye adzagumulapo, monga mbiya ya woumba isweka, ndi kuiswaiswa osaileka; ndipo sipadzapezedwa m'zigamphu zace phale lopalira moto pacoso, ngakhale lotungira madzi padziwe.

15 Pakuti atero Ambuye, Yehova Woyera wa Israyeli, M'kubwera ndi m'kupuma inu mudzapulumutsidwa; m'kukhala cete ndi m'kukhulupirira mudzakhala mphamvu yanu; ndipo simunafuna.

16 Koma munati, Iai, pakuti tidzathawa pa akavalo; cifukwa cace inu mudzathawadi; ndipo ife tidzakwera pa akavalo aliwiro; cifukwa cace iwo amene akuthamangitsani, adzakhala aliwiro.

17 Cikwi cimodzi cidzathawa pakuwadzudzula mmodzi; pakukudzudzulani anthu asanu mudzathawa; kufikira inu mudzasiyidwa ngati mlongoti pamwamba pa phiri, ndi ngati mbendera pamwamba pa citundu.

18 Cifukwa cace Yehova adzadikira, kuti akukomereni mtima, ndipo cifukwa cace Iye adzakuzidwa, kuti akucitireni inu cifundo; pakuti Yehova ndiye Mulungu wa ciweruziro; odala ali onse amene amdikira Iye.

19 Pakuti anthu adzakhala m'Ziyoni pa Yerusalemu; iwe sudzaliranso, Iye ndithu adzakukomera mtima pakumveka kupfuula kwako; pakumva Iye adzayankha.

20 Ndipo ngakhale Ambuye adzakupatsani inu cakudya ca nsautso, ndi madzi a cipsinjo, koma aphunzitsi ako sadzabisikanso, koma maso ako adzaona aphunzitsi ako;

21 ndipo makutu ako adzamva mau kumbuyo kwa iwe akuti, Njira ndi iyi, yendani inu m'menemo: potembenukira inu kulamanja, ndi potembenukira kulamanzere.

22 Ndipo mudzaipitsa cokuta ca mafano ako, osema asiliva, ndi comata ca mafano ako osungunula agolidi; udzawataya ngati kanthu konyansa, udzati kwa iwo, Cokani.

23 Ndipo Mulungu adzapatsa mvula ya mbeu yako, ukaibzale m'nthaka; ndi mkate ndiwo phindu la nthaka, ndipo tirigu wace adzaca bwino ndi kucuruka; tsiku limenelo ng'ombe zako zidzadya m'madambo akuru.

24 Momwemonso ng'ombe ndi ana a buru olima nthaka adzadya cakudya cocezera, cimene capetedwa ndi cokokolera ndi mkupizo.

25 Ndipo pamwamba pa mapiri akuru onse, ndipa zitunda zonse zazitaritari padzakhala mitsinje ndi micerenje ya madzi, tsiku lophana lalikuru, pamene nsanja zidzagwa.

26 Komanso kuwala kwace kwa mwezi kudzakhala ngati kuwala kwa dzuwa, ndi kuwala kwa dzuwa kudzakula monga madzuwa asanu ndi awiri, monga kuwala kwa masiku asanu ndi awiri, tsiku limenelo Yehova adzamanga bala la anthu ace, nadzapoletsa khana limene anawakantha ena.

27 Taonani, dzina la Yehova licokera kutari, mkwiyo wace uyaka, malawi ace ndi akuru; milomo yace iri yodzala ndi ukali, ndi lilime lace liri ngati moto wonyambita;

28 ndi mpweya wace uli ngati mtsinje wosefukira, umene ufikira m'khosi, kupeta mitundu ya anthu ndi copetera ca cionongeko; ndi capakamwa calakwitsa, cidzakhala m'nsagwada za anthu.

29 Inu mudzakhala ndi nyimbo, monga usiku, podya phwando lopatulika; ndi mtima wokondwa, monga pomuka wina ndi citoliro, kufikira ku phiri la Yehova, ku thanthwe la Israyeli,

30 Ndipo Yehova adzamveketsa mau ace a ulemerero, ndipo adzaonetsa kumenya kwa dzanja lace, ndi mkwiyo wace waukali, ndi lawi la moto wonyambita, ndi kuomba kwa mphepo, ndi mkuntho ndi matalala.

31 Pakuti ndi mau a Yehova Asuri adzatyokatyoka, ndi ndodo yace adzammenya.

32 Ndipo nthawi zonse Yehova adze vakantha ndi ndodo yosankhikayo, padzamveka mangaka ndi zeze; ndi m'nkhondo zothunyana-thunyana, Iye adzamenyana nao.

33 Pakuti Tofeti wakonzedwa kale, inde cifukwa ca mfumu wakonzedweratu; Iye wazamitsapo, nakuzapo; mulu wacewo ndi moto ndi nkhuni zambiri; mpweya wa Yehova uuyatsa ngati mtsinje wasulfure.

31

1 Tsoka kwa iwo amene atsikira kunka ku Aigupto kukathandizidwa, natama akavalo; nakhulupirira magareta, pakuti ali ambiri, ndi okwera pa akavalo, pakuti ali a mphamvu zambiri; koma sayang'ana Woyera wa Israyeli, ngakhale kumfuna Yehova!

2 Koma Iyenso ali wanzeru, nadzatengera coipa, ndipo sadzabwezanso mau ace, koma adzaukira banja la ocita zoipa, ndi amene athandiza iwo akugwira nchito yoipa.

3 Koma Aaigupto ndiwo anthu, si Mulungu; ndi akavalo ao ali nyama, si mzimu; ndipo pamene Yehova adzatambasula dzanja lace, wothandiza adzapunthwa, ndi wothandizidwa adzagwa, ndipo iwo onse awiri pamodzi adzalephera.

4 Pakuti Yehova atero kwa ine, Monga mkango, ndi mwana wa mkango wobangula pa nyama yace, sudzaopa mau a khamu la abusa oitanidwa kuupitikitsa, ngakhale kudzicepetsa wokha, cifukwa ca phokoso lao; motero Yehova wa makamu adzatsikira kumenyana nkhondo ku phiri la Ziyoni, ndi kucitunda kwace komwe.

5 Monga mbalame ziuluka, motero Yehova wamakamu adzacinjiriza Yerusalemu; Iye adzacinjirikiza ndi kuupulumutsa, adzapitirapo ndi kuusunga.

6 Bwerani kwa Iye amene mwampandukira kolimba, ana a Israyeli inu.

7 Pakuti tsiku limenelo iwo adzataya munthu yense mafano ace asiliva, ndi mafano ace agolidi amene manja anu anu anawapanga akucimwitseni inu.

8 Pamenepo Asuri adzagwa ndi lupanga losati la munthu; ndi lupanga losati la anthu lidzammariza iye; ndipo iye adzathawa lupanga, ndi anyamata ace adzalamba.

9 Ndipo mwala wace udzacoka, cifukwa ca mantha, ndi akalonga ace adzaopa mbendera, ati Yehova, amene moto wace uli m'Ziyoni, ndi ng'anjo yace m'Yerusalemu.

32

1 Taonani mfumu idzalamulira m'cilungamo, ndi akalonga adzalamulira m'ciweruzo.

2 Ndipo munthu adzakhala monga pobisalira mphepo, ndi pousira cimphepo; monga mitsinje yamadzi m'malo ouma, monga mthunzi wa thanthwe lalikuru m'dziko lotopetsa.

3 Ndipo maso a iwo amene aona sadzatsinzina, ndi makutu a iwo amene amva adzamvera.

4 Mtimanso wansontho udzadziwa nzeru, ndi lilume la acibwibwi lidzalankhula zomveka msanga.

5 Wopusa sadzayesedwanso woolowa manja, ngakhale wouma manja sadzayesedwa mfulu.

6 Pakuti wopusa adzanena zopusa, ndi mtima wace udzacita mphulupulu, kucita zoipitsa, ndi kunena za Yehova molakwira, kusowetsa konse mtima wanjala, ndi kulepheretsa cakumwa ca waludzu.

7 Zipangizonso za womana ziri zoipa; iye apangira ziwembu zakuononga waumphawi ndi mau onama, ngakhale pamene wosowa alankhula zoona.

8 Koma mfulu aganizira zaufulu, nakhazikika m'zaufulu zomwe.

9 Ukani, akazi inu, amene mulinkukhala phe, mumve mau anga; mu ana akazi osasamalira, cherani makutu pa kulankhula kwanga.

10 Pakutha caka, kudza masiku ena inu mudzabvutidwa, inu akazi osasamalira; pakuti masika a mphesa adzasoweka, sadzatuta konse.

11 Nthunthumirani, inu akazi, amene mulinkukhalaphe; bvutidwani, inu osasamalira, bvulani mukhale marisece, nimumange ciguduli m'cuuno mwanu.

12 Iwo adzadzimenya pazifuwa cifukwa ca minda yabwino, cifukwa ca mpesa wobalitsa.

13 Pa dziko la anthu anga padzafika minga ndi lunguzi; inde pa nyumba zonse zokondwa, m'mudzi wokondwerera;

14 pakuti nyumba ya mfumu idzasiyidwa; mudzi wa anthu ambiri udzakhala bwinja; citunda ndi nsanja zidzakhala nkhwimba ku nthawi zonse, pokondwera mbidzi podyera zoweta;

15 kufikira mzimu udzathiridwa pa ife kucokera kumwamba, ndi cipululu cidzasanduka munda wobalitsa, ndi munda wobalitsa udzayesedwa nkhalango.

16 Pamenepo ciweruzo cidzakhala m'cipululu, ndi cilungamo cidzakhala m'munda wobalitsa.

17 Ndi nchito ya cilungamo idzakhala mtendere; ndi zotsata cilungamo zidzakhala mtendere, ndi kukhulupirika ku nthawi zonse.

18 Ndipo anthu anga adzakhala m'malo a mtendere, ndi mokhala mokhulupirika ndi mopuma mwa phe.

19 Koma kudzagwa matalala m'kugwa kwace kwa nkhalango; ndipo mudzi udzagwetsedwa ndithu.

20 Odala muli inu, amene mubzala m'mbali mwa madzi monse, amene muyendetsa mapazi a ng'ombe ndi buru.

33

1 Tsoka kwa iwe amene usakaza, cinkana sunasakazidwa; nupangira ciwembu, cinkana sanakupangira iwe ciwembu! Utatha kusakaza, iwe udzasakazidwa; ndipo utatha kupangira ciwembu, iwo adzakupangira iwe ciwembu.

2 Inu Yehova, mutikomere ife mtima; ife talindira Inu; mukhale dzanja lathu m'mawa ndi m'mawa, cipulumutso cathunso m'nthawi ya mabvuto.

3 Pa mau a phokoso mitundu ya anthu yathawa; ponyamuka iwe amitundu abalalika,

4 Ndipo zofunkha zanu zidzasonkhanitsidwa, monga ziwala zisonkhana; monga madzombe atumpha, iwo adzatumpha pa izo.

5 Yehova wakwezedwa; pakuti akhala kumwamba; Iye wadzaza Ziyoni ndi ciweruzo ndi cilungamo.

6 Ndipo kudzakhala cilimbiko m'nthawi zako, cipulumutso cambiri, nzeru ndi kudziwa; kuopa kwa Yehova ndiko cumacace.

7 Taonani, olimba mtima ao angopfuula kunja, mithenga ya mtendere ilira kowawa.

8 Njira zamakwalala zikufa, kulibe woyendamo; Asuri watyola cipangano, wanyoza midzi, sasamalira anthu.

9 Dziko lilira maliro ndi kulefuka; Lebano ali ndi manyazi, nafota; Saroni afanana ndi cipululu; pa Basana ndi Karimeli papukutika.

10 Tsopano ndidzauka, ati Yehova; tsopano ndidzanyamuka, tsopano ndidzakwezedwa.

11 Inu mudzatenga pakati ndi mungu, mudzabala ziputu; mpweya wanu ndi moto umene udzakumarizani inu.

12 Ndipo mitundu ya anthu idzanga potentha miyala yanjeresa; monga minga yodulidwa, nitenthedwa ndi moto.

13 Imvani inu amene muli kutari, cimene ndacita ndi inuamene muli pafupi, bvomerezani mphamvu zanga,

14 Ocimwa a m'Ziyoni ali ndi mantha, kunthunthumira kwadzidzimutsa anthu opanda Mulungu. Ndani mwa ife adzakhala ndi moto Wakunyeketsa? ndani mwa ife adzakhala ndi zotentha zacikhalire?

15 Iye amene ayenda molungama, nanena molunjika; iye amene anyoza phindu lonyenga, nasansa manja ace kusalandira zokometsera milandu, amene atseka makutu ace kusamva za mwazi, natsinzina maso ace kusayang'ana coipa;

16 iye adzakhala pamsanje; malo ace ocinjikiza adzakhala malinga amiyala; cakudya cace cidzapatsidwa kwa iye; madzi ace adzakhala cikhalire.

17 Maso ako adzaona mfumu m'kukongola kwace; iwo adzaona dziko lakutari.

18 Mtima wako udzaganizira zoopsya; mlembi ali kuti? ali kuti iye amene anayesa msonkho? ali kuti iye amene anawerenga nsanja?

19 Iwe sudzaona anthu aukali, anthu a mau anthulu, amene iwe sungazindikire; a lilume lacibwibwi, limene iwe sungalimve.

20 Tayang'ana pa Ziyoni, mudzi wa mapwando athu; maso ako adzaona Yerusalemu malo a phe, cihema cimene sicidzasunthidwa, ziciri zace sizidzazulidwa konse, zingwe zace sizidzadulidwa.

21 Koma pamenepo Yehova adzakhala ndi ife m'cifumu, malo a nyanja zacitando ndi mitsinje; m'menemo ngalawa sizidzayenda ndi ngombo, ngakhale zombo zazikuru sizidzapita pamenepo.

22 Pakuti Yehova ndiye woweruza wathu, Yehova ndiye wotipatsa malamulo, Yehova ndiye mfumu yathu; Iye adzatipulumutsa.

23 Zingwe zako za ngalawa zamasulidwa; sizinathe kulimbitsa patsinde pa mlongoti wace, sizinathe kufutukula matanga; pamenepo ndipo colanda cacikulu, cofunkha cinagawanidwa; wopunduka nafumfula.

24 Ndipo wokhalamo sadzanena, Ine ndidwala; anthu okhala m'menemo, adzakhululukidwa mphulupulu zao.

34

1 Idzani pafupi, amitundu inu, kuti mumve; mverani anthu inu, dziko limve, ndi za mommo; dziko ndi zinthu zonse zoturukamo.

2 Pakuti Yehova akwiyira amitundu onse, nacitira ukali khamu lao lonse; Iye wawaononga psiti, wawapereka kukaphedwa,

3 Ophedwa aonso adzatayidwa kunja, ndipo kununkha kwa mitembo yao kudzamveka, ndipo mapiri adzasungunuka ndi mwazi wao.

4 Ndipo makamu onse a kumwamba adzasungunuka, ndi miyamba idzapindika pamodzi ngati mpukutu; makamu ao onse adzafota monga tsamba limafota pampesa ndi kugwa, ndi monga tsamba lifota pamkuyu.

5 Pakuti lupanga langa lakhuta kumwamba; taonani, lidzatsikira pa Edomu, ndi pa anthu amene ndawatemberera, kuti aweruzidwe.

6 Lupanga la Yehova lakhuta ndi mwazi, lanona ndi mafuta ndi mwazi wa ana a nkhosa, ndi mbuzi, ndi mafuta a imso ya nkhosa zamphongo; pakuti Yehova ali ndi nsembe m'Bozira, ndi ophedwa ambiri m'dziko la Edomu.

7 Ndipo njati zidzatsika ndi iwo, ndi ng'ombe zofula ndi zamphongo; ndi dziko lao lidzakhuta ndi mwazi, ndi pfumbi lao lidzanona ndi mafuta.

8 Pakuti liri tsiku la kubwezera la Yehova, caka cakubwezera cilango, mlandu wa Ziyoni.

9 Ndipo mitsinjeyo idzasanduka matope akuda, ndi pfumbilo lidzasanduka suifure, ndi dziko lacelo lidzasanduka matope oyaka moto.

10 Sadzazimikai usiku, ngakhale usana; utsi wace udzakwera nthawi zonse; m'mibadwo mibadwo lidzakhala labwinja, palibe amene adzapitapo nthawi za nthawi.

11 Koma bvuo ndi nungu zidzakhalamo, ndipo kadzidzi ndi khungubwi adzakhala m'menemo, ndipo Mulungu adzatambalika pamenepo cingwe coongolera ca cisokonezo, ndi cingwe colungamitsa ciriri cosatha kucita kanthu.

12 Iwo adzaitana mfulu zace zilowe m'ufumu, koma sizidzaonekako; ndi akalonga ace onse adzakhala cabe.

13 Ndipo minga idzamera m'nyumba zace zazikuru, khwisa ndi mitungwi m'malinga mwace; ndipo adzakhala malo a ankhandwe, ndi bwalo la nthiwatiwa.

14 Ndipo zirombo za m'cipululu zidzakomana ndi mimbulu, tonde adzaitana mnzace; inde mancici adzatera kumeneko, nadzapeza popumira.

15 Kumeneko njoka yotumpha idzapanga cisanja cace, niikira, niumatira, niswa mumthunzi mwace; inde kumeneko miimba idzasonkhana wonse ndi unzace.

16 Funani inu m'buku la Yehova, nimuwerenge; palibe umodzi wa iye udzasowa, palibe umodzi udzasowa unzace; pakuti pakamwa pa Yehova panena, ndipo mzimu wace wasonkhanitsa iwo.

17 Ndipo Iye wacita maere, cifukwa ca zirombozi, ndipo dzanja lace lazigawira dzikolo ndi cingwe, zidzakhala nalo nthawi zonse ku mibadwo mibadwo, zidzakhala m'menemo.

35

1 Cipululu ndi malo ouma adzakondwa; ndipo dziko loti se lidzasangalala ndi kuphuka ngati duwa.

2 Lidzaphuka mocuruka ndi kusangalala, ngakhale kukondwa ndi kuyimba; lidzapatsidwa ulemerero wa Lebano, ndi ukuru wa Karimeli ndi Saroni; anthuwo adzaona ulemerero wa Yehova, ukuru wace wa Mulungu wathu.

3 Limbitsani manja opanda mphamvu, ndi kulimbitsa maondo a gwedegwede.

4 Nenani kwa a mitima ya cinthenthe, Limbani, musaope; taonani, Mulungu wanu adza ndi kubwezera cilango, ndi mphotho ya Mulungu; Iye adzafika ndi kukupulumutsani.

5 Pamenepo maso a akhungu adzatsegudwa, ndi makutu a ogontha adzatsegulidwa.

6 Pamenepo wopunduka adzatumpha ngati nswala, ndi lilume la wosalankhula lidzayimba; pakuti m'cipululu madzi adzaturuka, ndi mitsinje m'dziko loti se.

7 Ndipo mcenga wong'azimira udzasanduka thamanda, ndi nthaka yopanda madzi idzasanduka zitsime zamadzi; m'malo a ankhandwe m'mene iwo anagona, mudzakhala udzu ndi mabango ndi milulu.

8 Ndipo kudzakhala khwalala kumeneko, ndi njira, ndipo idzachedwa njira yopatulika; audio sadzapita m'menemo; koma Iye adzakhala nao oyenda m'njira, ngakhale opusa, sadzasocera m'menemo.

9 Sikudzakhala mkango kumeneko, ngakhale cirombo colusa sicidzapondapo, pena kupezedwa pamenepo; koma akuomboledwa adzayenda m'menemo,

10 ndiro oomboledwa a Yehova adzabwera, nadzafika ku Ziyoni alikuyimba; kukondwa kosatha kudzakhala pa mitu yao; iwo adzakhala ndi kusekerera ndi kukondwa, ndipo cisoni ndi kuusa moyo kudzacoka.

36

1 Koma panali caka cakhumi ndi cinai ca mfumu Hezekiya, Sanakeribu, mfumu ya Asuri anadza, nathira nkhondo pa midzi ya malinga yonse ya Yuda, nailanda.

2 Ndipo mfumu ya Asuri inatumiza kazembe kucokera pa Lakisi, kunka ku Yerusalemu, kwa mfumu Hezekiya, ndi nkhondo yambiri. Ndipo iye anaima cifupi ndi mcerenje wa thamanda la kumtunda, m'khwalala la pa mwaniko wa wotsuka nsaru.

3 Ndipo anamturukira Eliakimu, mwana wa Hilikiya, amene anali wapanyumba, ndi Sebina, mlembi, ndi Yoaki, mwana wa Asafu, mkumbutsi.

4 Ndipo kazembeyo anati kwa iwo, Nenani inu tsopano kwa Hezekiya, Itero mfumu yaikuru, mfumu ya Asuri, Kodi cikhulupiriro ici ncotani, ucikhulupirira iwe?

5 Ine nditi, Uphungu wako, ndi mphamvu zako za kunkhondo, zingokhala mau acabe; tsopano ukhulupirira yani, kuti wandipandukira ine?

6 Taona, ukhulupirira ndodo yabango iyi yophwanyika, kunena Aigupto; imene munthu akaitsamira, idzalowa m'dzanja mwace, ndi kulipyoza; momwemo Farao, mfumu ya Aigupto, kwa onse amene amkhulupirira iye.

7 Koma ukanena kwa ine, Ife tikhulupirira Yehova Mulungu wathu; kodi si ndiye amene Hezekiya wacotsa misanje yace ndi maguwa ace a nsembe, nati kwa Yuda, ndi kwa Yerusalemu, Inu mudzapembedzera patsogolo pa suwa la nsembe ili?

8 Cifukwa cace upereketu zikole kwa mbuyanga, mfumu ya Asuri, ndipo ine ndidzakupatsa iwe akavalo zikwi ziwiri, ngati iwe udzaona okwerapo.

9 Bwanji tsono iwe ungathe kubweza nkhope ya nduna mmodzi wamng'ono wa atumiki a mbuyanga, ndi kukhulupirira Aigupto, kuti adzakupatsa magareta ndi apakavalo?

10 Ndipo ine tsopano, kodi ndafika opanda Yehova kudzamenyana ndi dziko ili, kudzalipasula? Yehova anati kwa ine, Kwera, ndi kumenyana ndi dziko ili, ndi kulipasula.

11 Ndipo Eliakimu, ndi Sebina, ndi Yoaki, anati kwa kazembeyo, Nenanitu kwa atumiki anu m'cinenero ca Aramu; pakuti ife ticimva; ndipo musanene kwa ife m'Ciyuda, m'makutu a anthu amene ali palinga.

12 Koma kazembeyo anati, Kodi mbuyanga ananditumiza ine kwa mbuyako ndi kwa iwe kunena mau amenewa? kodi iye sananditumiza ine kwa amuna okhala palinga, kuti adye ndowe zao zao, ndi kumwa madzi ao ao ndi inu?

13 Pamenepo kazembeyo anaima, napfuula ndi mau akuru m'Ciyuda, nati, Imvani, inu, mau a mfumu yaikuru, mfumu ya Asuri.

14 Mfumu itere, Musaleke Hezekiya anyenge inu; pakuti iye sadzathai kukupulumutsani:

15 ngakhale musaleke Hezekiya akhulupiritse inu kwa Yehova, ndi kunena, Yehova adzatipulumutsa ndithu; mudzi uwu sudzaperekedwa m'manja mwa mfumu ya Asuri.

16 Musamvere Hezekiya, pakuti mfumu ya ku Asuri itere, Mupangane nane, turukirani kwa ine; ndipo yense adye mphesa zace, ndi nkhuyu zace, namwe yense madzi a pa citsime cace;

17 kufikira ine ndidzadza, ndi kunka nanu ku dziko lofanana ndi lanu, dziko la tirigu ndi vinyo, dziko la cakudya ndi minda yamphesa.

18 Cenjerani angakukopeni inu Hezekiya, ndi kuti, Yehova adzatipulumutsa ife. Kodi milungu iri yonse ya amitundu inapulumutsa dziko lao m'manja mwa mfumu ya ku Asuri?

19 Iri kuti milungu ya Hamati, ndi Aripadi? iri kuti milungu ya Sefaravaimu? kodi inapulumutsa Samariya m'manja mwanga?

20 Mwa milungu yonse ya maiko awa, inapulumutsa dziko lao m'manja mwanga ndi iti, kuti Yehova adzapulumutsa Yerusalemu m'manja mwanga?

21 Koma iwo anakhala cete, osamuyankha mau, pakuti mfumu inawalamulira kuti, Musamuyankhe.

22 Ndipo anafika Eliakimu, mwana wa Hilikiya, amene anali wapanyumba, ndi Sebina, mlembi, ndi Yoaki, mwana wa Asafu, mkumbutsi, kwa Hezekiya ndi zobvala zao zong'ambika, namuuza iye mau a kazembeyo.

37

1 Ndipo panali pamene mfumu Hezekiya anamva, anang'amba zobvala zace, nabvala ciguduli, nalowa m'nyumba ya Yehova.

2 Ndipo anatumiza Eliakimu, wapanyumba, ndi Sebina, mlembi, ndi akuru a nsembe, atapfunda ciguduli, kwa Yesaya, mneneri, mwana wa Amozi.

3 Ndipo iwo anati kwa iye, Hezekiya atere, Tsiku lalero ndilo tsiku la bvuto, ndi lakudzudzula, ndi citonzo; pakuti nthawi yace yakubala ana yafika, ndipo palibe mphamvu yobalira.

4 Kapena Yehova Mulungu wako adzamva mau a kazembeyo, amene mfumu ya Asuri mbuyace inamtuma kukatonza Mulungu wamoyo, nadzadzudzula mau amene Yehova Mulungu wako adawamva; cifukwa cace, kweza pemphero lako cifukwa ca otsala osiyidwa.

5 Ndipo atumiki a mfumu Hezekiya anadza kwa Yesaya.

6 Ndipo Yesaya anati kwa iwo, Mukati kwa mbuyanu, Atero Yehova, musaope mau amene wawamva iwe, amene atumiki a mfumu ya Asuri andilalatira Ine.

7 Taonani, ndidzaika mzimu mwa iye, ndipo iye adzamva mbiri, nadzabwerera kunka ku dziko la kwao; ndipo ndidzamgwetsa ndi lupanga m'dziko la kwao.

8 Ndipo kazembeyo anabwerera, napeza mfumu ya Asuri irikuponyana nkhondo ndi Libina; pakuti anamva kuti inacoka ku Lakisi.

9 Ndipo anamva anthu alinkunena za Tiraka, mfumu ya Kusi, Iye waturuka kudzamenyana ndi iwe. Ndipo pamene anamva, iye anatumiza mithenga kwa Hezekiya ndi kuti,

10 Mukati kwa Hezekiya, mfumu ya Yuda, Asakunyenge Mulungu wako, amene iwe umkhulupirira, ndi kuti, Yerusalemu sadzaperekedwa m'manja mwa mfumu ya Asuri.

11 Taona, iwe wamva cimene mafumu a Asuri anacitira maiko onse, ndi kuwapasula konse; ndipo kodi iwe udzapulumutsidwa?

12 Kodi milungu ya amitundu yaipulumutsa iyo, imene atate anga anaipasula? Gozani ndi Harani ndi Rezefi ndi ana a Edeni amene anali m'Telasara.

13 Iri kuti mfumu ya ku Hamati, ndi mfumu ya ku Aripadi, ndi mfumu yamudzi wa ku Sefaravaimu, ya ku Hena, ndi Iveva?

14 Ndipo Hezekiya analandira kalatayo m'manja mwa mithengayo, namuwerenga; ndipo Hezekiya anakwera kunka ku nyumba ya Yehova, namfunyulula pamaso pa Yehova.

15 Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova, nati,

16 Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli, amene mukhala pa akerubi, Inu ndinu Mulungu, Inu nokha, wa maufumu onse a dziko lapansi, Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

17 Cherani makutu anu, Yehova, nimumve; tsegulani maso anu, Yehova, nimuone; ndi kumva mau onse a Sanakeribu, amene watumiza kumtonza Mulungu wamoyo.

18 Zoonadi, Yehova, mafumu a Asuri anaononga maiko onse, ndi pokhala pao.

19 Ndipo anaponya milungu yao pamoto; pakuti iyo sinali milungu, koma nchito yopangidwa ndi manja a anthu, mtengo ndi mwala; cifukwa cace iwo anaiononga,

20 Cifukwa cace, Yehova, Mulungu wathu, mutipulumutse ife m'manja mwace, kuti maufumu onse a dziko adziwe, kuti Inu ndinu Yehova, Inu nokha.

21 Ndipo Yesaya, mwana wa Amozi, anatumiza kwa Hezekiya, ndi kuti, Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli, Popeza wandipemphera za Sanakeribu mfumu ya Asuri,

22 awa ndiwo mau amene Yehova wanena za iye, Namwali, mwana wamkazi wa Ziyoni, wakunyoza iwe ndi kuseka iwe ndi ciphwete; mwana wamkazi wa Yerusalemu wapukusa mutu wace pambuyo pako.

23 Ndani amene, iwe wamtonza ndi kumlalatira? ndani amene iwe wakwezera mau ako ndi kutukulira maso ako kumwamba? ndiye Woyera wa Israyeli.

24 Wamtonza Ambuye ndi atumiki ako, ndipo wati, Ndi khamu la magareta anga ine ndafika ku nsonga za mapiri, ku mbali za Lebano; ndipo ndidzagwetsapo mikungudza yaitali, ndi milombwa yosankhika; ndipo ine ndidzafika pamutu pace penipeni, ku nkhalango ya munda wace wobalitsa.

25 Ine ndakumba ndi kumwa madzi, ndidzaumitsa nyanja zonse za Aigupto ndi kuphazi kwanga.

26 Kodi iwe sunamve, kuti ndinacita ici kale, ndi kucikonza nthawi zakale? tsopano Ine ndacikwaniritsa, kuti iwe ukapasule midzi yamalinga, isanduke miunda.

27 Cifukwa cace okhalamo analefuka, naopsedwa, nathedwa nzeru; ananga udzu wa in'munda, ndi masamba awisi, ndi udzu wa pamacindwi, ndi munda wa tirigu asanakule.

28 Koma ndidziwa pokhala pansi pako, ndi kuturuka kwako, ndi kulowa kwako, ndi kundikwiyira kwako.

29 Cifukwa ca kundikwiyira Ine kwako, ndi popeza kudzikweza kwako kwafika m'makutu mwanga. Ine ndidzaika mbedza yanga m'mphuno mwako, ndi capakamwa canga m'milomo yako, ndipo ndidzakubweza iwe m'njira yomwe unadzerayo.

30 Ndipo ici cidzakhala cizindikilo kwa iwe: caka cino mudzadya zimene ziri zomera zokha, ndipo caka caciwiri mankhokwe ace; ndipo caka cacitatu bzalani ndi kudula ndi kulima minda yamphesa ndi kudya cipatso cace.

31 Ndipo otsala amene opulumuka a nyumba ya Yuda adzaphukanso mizu pansi, nadzabala cipatso pamwamba.

32 Pakuti mudzaoneka m'Yerusalemu, otsala ndi opulumuka m'Yerusalemu, otsala ndi opulumuka m'phiri la Ziyoni; cangu ca Yehova wa makamu cidzacita ici.

33 Cifukwa cace atero Yehova za mfumu ya Asuri, Iye sadzafika pa mudzi uno, ngakhale kuponyapo mubvi, ngakhale kufika patsogolo pace ndi cikopa, ngakhale kuunjikirapo mulu.

34 Pa njira yomwe anadzerayo, abwerera yomweyo, ndipo sadzafika pa mudzi uno, ati Yehova.

35 Pakuti ndidzacinjiriza mudzi uno, kuupulumutsa, cifukwa ca Ine mwini, ndi mtumiki wanga Davide.

36 Ndipo mthenga wa Yehova anaturuka, naphaipha m'zitando za Asuri, zikwi zana ndi makumi asanu ndi atatu ndi zisanu, ndipo pamene anthu anauka mamawa, taonani, onse ndiwo mitembo.

37 Ndipo Sanakeribu, mfumu ya Asuri, anacoka, namuka, nabwerera, nakhala pa Nineve,

38 Ndipo panali, pamene iye analikupembedzera m'nyumba ya Nisiroki, mulungu wace, Adrameleki ndi Sarezeri, ana ace anampha iye ndi lupanga; ndipo iwo anapulumuka, nathawira ku dziko la ku Ararati. Ndipo Esaradoni, mwana wace, analamulira m'malo mwace.

38

1 Masiku amenewo Hezekiya anadwala, nafuna kufa. Ndipo Yesaya mneneri, mwana wa Amozi, anadza kwa iye, nati kwa iye, Atero Yehova, Konza nyumba yako, pakuti iwe udzafa, sudzakhala ndi moyo.

2 Ndipo Hezekiya analoza nkhope yace kukhoma, napemphera kwa Yehova, nati,

3 Kumbukiranitu tsopano, Yehova, kuti ndayenda pamaso panu m'zoonadi ndi mtima wangwiro, ndipo ndacita zabwino pamaso panu. Ndipo Hezekiya analira kolimba.

4 Ndipo anafika mau a Yehova kwa Yesaya, ndi kuti,

5 Ukanene kwa Hezekiya, Atero Yehova, Mulungu wa Davide, kholo lako, Ndamva kupemphera kwako, ndaona misozi yako; taona, ndidzaonjezera pa masiku ako zaka khumi ndi zisanu.

6 Ndipo ndidzakupulumutsa iwe ndi mudzi uno m'manja mwa mfumu ya Asuri, ndipo ndidzacinjiriza mudzi uno.

7 Ndipo ici cidzakhala cizindikilo kwa iwe cocokera kwa Yehova, kuti Yehova adzacita ici wanenaci;

8 taona, ndidzabweza mthunzi wa pamakwerero, umene watsika pa makwerero a Ahazi ndi dzuwa, ubwerere makwerero khumi. Ndipo dzuwa linabwerera makwerero khumi pamakwerero, pamene udatsika mthunziwo.

9 Malemba a Hezekiya mfumu ya Ayuda muja anadwala, atacira nthenda yace.

10 Ine ndinati, Pakati pa masiku anga ndidzalowa m'zipata za kunsi kwa manda; Ndazimidwa zaka zanga zotsala.

11 Ndinati, Sindidzaona Yehova m'dziko la amoyo; sindidzaonanso munthu pamodzi ndi okhala kunja kuno;

12 Pokhala panga pacotsedwa, pandisunthikira monga hema wambusa; Ndapindapinda moyo wanga ngati muomba; Iye adzandidula ine poomberapo; Kuyambira usana kufikira usiku mudzanditsiriza ine.

13 Ndinadzitonthoza kufikira mamawa; monga mkango, momwemo Iye anatyolatyola mafupa anga onse; Kuyambira usana kufikira usiku mudzanditsiriza ine.

14 Ndinalankhula-lankhula ngati namzeze, pena cumba; Ndinalira maliro ngati nkhunda; Maso anga analephera pogadamira kumwamba. Yehova ndasautsidwa, mundiperekere cikoli.

15 Kodi ndidzanena ciani? Iye wanena kwa ine, ndiponso Iye mwini wacita ici; Ine ndidzayenda cete zaka zanga zonse, Cifukwa ca zowawa za moyo wanga.

16 Ambuye ndi zinthu izi anthu akhala ndi moyo. Ndipo m'menemo monse muli moyo wa mzimu wanga; Cifukwa cace mundiciritse ine, Ndi kundikhalitsa ndi moyo.

17 Taonani, ndinali ndi zowawa zazikuru, Cifukwa ca mtendere wanga; Koma Inu mokonda moyo wanga, Munaupulumutsa m'dzanja la cibvundi, Pakuti mwaponya m'mbuyo mwanu macimo anga onse.

18 Pakuti kunsi kwa manda sikungakuyamikeni Inu; Imfa singakulemekezeni; Otsikira kudzenje sangaziyembekeze zoona zanu.

19 Wamoyo, wamoyo, iye adzakuyamikani inu, monga ine lero; Atate adzadziwitsa ana ace zoona zanu.

20 Yehova ndiye wondipulumutsa ine; Cifukwa cace tidzayimba nyimbo zanga, ndi zoyimba zazingwe Masiku onse a moyo wathu m'nyumba ya Yehova.

21 Ndipo Yesaya adati, Atenge mbulu wankhuyu, auike papfundo, Ndipo iye adzacira.

22 Hezekiya anatinso, Cizindikilo nciani, kuti ndidzakwera kunka ku nyumba ya Yehova?

39

1 Nthawi imeneyo Merodakibaladani, mwana wa Baladani, mfumu ya ku Babulo, anatumiza akalata ndi mphatso kwa Hezekiya; pakuti anamva kuti iye anadwala, nacira.

2 Ndipo Hezekiya anakondwera nao, nawaonetsa nyumba yace ya cuma, siliva, ndi golidi, ndi zonunkhira, ndi mafuta okometsetsa, ndi nyumba yonse ya zida zace, ndi zonse zopezedwa m'zosungira zace; munalibe kanthu m'nyumba mwace, kapena m'dziko lace lonse, kamene Hezekiya sanawaonetsa.

3 Ndipo anadza Yesaya mneneri kwa mfumu Hezekiya, nati kwa iye, Kodi anthu awa ananena bwanji, ndipo iwo acokera kuti, kudza kwa inu? Ndipo Hezekiya anati, Iwo acokera ku dziko lakutari, kudza kwa ine, kunena ku Babulo.

4 Ndipo iye anati, Kodi iwo anaona ciani m'nyumba mwanu? Ndipo Hezekiya anayankha, Zonse za m'nyumba mwanga iwo anaziona; palibe kanthu ka mwa cuma canga, kamene ine sindinawaonetse.

5 Ndipo Yesaya anati kwa Hezekiya, Imvani mau a Yehova wa makamu.

6 Taona, masiku afika, kuti zonse za m'nyumba mwako, ndi zimene atate ako anazikundika kufikira lero lino, zidzatengedwa kunka ku Babulo; sipadzatsala kanthu, ati Yehova.

7 Ndipo ana ako amene adzabadwa ndi iwe, amene udzabala, iwo adzawatenga, ndipo adzakhala adindo m'cinyumba cace ca mfumu ya ku Babulo.

8 Ndipo Hezekiya anati kwa Yesaya, Mau a Yehova, amene iwe wanena, ali abwino. Iye anatinso, Pakuti padzakhala mtendere ndi zoonadi masiku anga.

40

1 Mutonthoze, mutonthoze mtima wa anthu anga, ati Mulungu wanu.

2 Munene inu zotonthoza mtima kwa Yerusalemu, nimupfuulire kwa iye, kuti nkhondo yace yatha, kuti kuipa kwace kwakhululukidwa; kuti iye walandira mowirikiza m'dzanja la Yehova, cifukwa ca macimo ace onse.

3 Mau a wopfuula m'cipululu, Konzani njira ya Yehova, lungamitsani m'dziko loti se khwalala la Mulungu wathu.

4 Cigwa ciri conse cidzadzazidwa, ndipo phiri liri lonse ndi citunda ciri conse zidzacepetsedwa, ndipo zokhota zidzaongoledwa, ndipo zamakolokoto zidzasalala;

5 ndipo ulemerero wa Yehova udzabvumbulutsidwa, ndipo anthu onse adzauona pamodzi, pakuti pakamwa pa Yehova panena comweco,

6 Mau a wina ati, Pfuula. Ndipo ndinati, Kodi ndipfuule ciani? Anthu onse ndi udzu, ndi kukoma kwao konse kunga duwa la m'thengo;

7 udzu unyala, duwa lifota; cifukwa mpweya wa Yehova waombapo; zoonadi anthu ndi udzu.

8 Udzu unyala, duwa lifota, koma mau a Mulungu wathu adzakhala nthawi zacikhalire.

9 Iwe amene utengera mau abwino ku Ziyoni, kwera iwe pamwamba pa phiri lalitari; iwe amene utengera mau abwino ku Yerusalemu, kweza mau ako ndi mphamvu, kwezetsa usaope, nena ku midzi ya Yuda, Taonani, Mulungu wanu!

10 Taonani, Ambuye Yehova adzadza ngati wamphamvu, ndipo mkono wace udzalamulira; taonani, mphoto yace iri ndi Iye, ndipo cobwezera cace ciri patsogolo pa Iye.

11 Iye adzadyetsa zoweta zace ngati mbusa, nadzasonkhanitsa ana a nkhosa pacapa pace, nadzawatengera pa cifuwa cace, ndipo adzatsogolera bwino bwino zimene ziyamwitsa.

12 Ndani wayesa madzi m'dzanja lace, nayesa thambo ndi cikhato, ndi kudzaza pfumbi la nthaka m'nsengwa, ndi kuyesa mapiri m'mbale zoyesera, ndi zitunda m'mulingo?

13 Ndani anapangira mzimu wa Yehova, kapena kukhala phungu lace, ndi kumphunzitsa Iye?

14 Iye anakhala upo ndi yani, ndipo ndani analangiza Iye ndi kumphunzitsa m'njira ya ciweruzo, ndi kumphunzitsa nzeru ndi kumuonetsa njira ya luntha?

15 Taonani, amitundu akunga dontho la m'mtsuko, nawerengedwa ngati pfumbi losalala la m'muyeso; taonani atukula zisumbu ngati kanthu kakang'ono.

16 Ndipo Lebano sakwanira kutentha, ngakhale nyama zace sizikwanira nsembe yopsereza.

17 Amitundu onse ali cabe pamaso pa Iye; awayesa ngati cinthu cacabe, ndi copanda pace,

18 Mudzafanizira Mulungu ndi yani tsopano, kapena kumyerekeza ndi cithunzithunzi cotani?

19 Pano losema mmisiri analisungunula, ndipo wosula golidi analikuta ndi golidi, naliyengera maunyolo asiliva.

20 Wosowa nsembe yoteroyo asankha mtengo umene sungabvunde, iye adzisankhira yekha munthu mmisiri waluso, akonze fano losema, limene silisunthika.

21 Kodi inu simunadziwe? kodi inu simunamve? kodi sanakuuzani inu ciyambire? kodi inu simunadziwitse ciyambire mayambiro a dziko lapansi?

22 Ndi Iye amene akhala pamwamba pa malekerezo a dziko lapansi, ndipo okhalamo akunga ziwala; amene afutukula thambo ngati cinsaru, naliyala monga hema wakukhalamo;

23 amene asandutsa akalonga kuti akhale acabe, nasandutsa oweruza a dziko lapansi akhale opanda pace,

24 Inde sanaokedwe, inde sanafesedwe; inde, muzu wao sunazike pansi; koma Iye anawaombetsera mphepo, ndipo afota, ndipo kabvumvulu awacotsa monga ciputu.

25 Mudzandifanizira Ine ndi yani tsono, kuti ndilingane naye, ati Woyerayo.

26 Kwezani maso anu kumwamba, muone amene analenga izo, amene aturutsa khamu lao ndi kuziwerenga; azicha zonse maina ao, ndi mphamvu zace zazikuru, ndi popeza ali wolimba mphamvu, palibe imodzi isoweka.

27 Bwanji iwe, Yakobo, umati, ndi bwanji umanena iwe, Israyeli, Njira yanga yabisika kwa Yehova; ndipo ciweruzo ca Mulungu wanga candipitirira?

28 Kodi iwe sunadziwe? kodi sunamve? Mulungu wacikhalire, Yehova, Mlengi wa malekezero a dziko lapansi, salefuka konse, salema; nzeru zace sizisanthulika.

29 Iye alimbitsa olefuka, naonjezera mphamvu iye amene alibe mphamvu.

30 Ngakhale anyamata adzalefuka ndi kulema ndi amisinkhu adzagwa ndithu:

31 koma iwo amene alindira Yehova adzatenganso mphamvu; adzauluka pamwamba ndi mapiko monga ziombankhanga; adzathamanga kuma osalema; adzayenda koma osalefuka.

41

1 Khalani cete pamaso pa Ine, zisumbu inu, anthu atengenso mphamvu; ayandikire; pamenepo alankhule; tiyeni, tiyandikire pamodzi kuciweruziro.

2 Ndani anautsa wina wocokera kum'mawa, amene amuitana m'cilungamo, afike pa phazi lace? Iye apereka amitundu patsogolo pace, namlamuliritsa mafumu; nawapereka monga pfumbi ku lupanga lace, monga ciputu couluzidwa ku uta wace.

3 Iye awathamangitsa, napitirira mwamtendere; pa njira imene asanapitemo ndi mapazi ace.

4 Ndani wacipanga, nacimariza ico, kuchula mibadwo ciyambire? Ine Yehova, ndine woyamba, ndi pacimariziro ndine ndemwe.

5 Zisumbu zinaona niziopa; malekezero a dziko lapansi ananthunthumira; anayandikira, nafika.

6 Iwo anathangata yense mnansi wace, ndi yense anati kwa mbale wace, Khala wolimba mtima.

7 Cotero mmisiri wa mitengo analimbikitsa wosula golidi, ndi iye amene asalaza ndi nyundo anamlimbikitsa iye amene amenya posulira, nanena za kulumikiza ndi nthobvu, Kuti kwabwino; ndipo iye akhomera fanolo misomali kuti lisasunthike.

8 Koma iwe, Israyeli, mtumiki wanga, Yakobo, amene ndinakusankha, mbeu ya Abrahamu bwenzi langa;

9 iwe amene ndinakuwira iwe zolimba kucokera ku malekezero a dziko lapansi, ndi kukuitana iwe kucokera m'ngondya zace, ndipo ndinati kwa iwe, Ndiwe mtumiki wanga ndakusankha, sindinakutaya kunja;

10 usaope, pakuti Ine ndiri pamodzi ndi iwe; usaopsyedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakucirikiza ndi dzanja langa lamanja la cilungamo.

11 Taona, onse amene akukwiyira iwe adzakhala ndi manyazi, nasokonezedwa; iwo amene akangana ndi iwe adzakhala ngati cabe, nadzaonongeka.

12 Iwe udzawafuna osawapeza, ngakhale iwo amene akangana ndi iwe; ocita nkhondo ndi iwe, adzakhala ngati cabe, ndi monga kanthu kopanda pace.

13 Pakuti Ine Yehova Mulungu wako ndidzagwira dzanja lako lamanja, ndi kunena kwa iwe, Usaope ndidzakuthandiza iwe.

14 Usaope, Yakobo, nyongolotsi iwe, ndi anthu inu a Israyeli; ndidzakuthangata iwe, ati Yehova, ndiye Mombolo wako, Woyera wa Israyeli.

15 Taona, ndidzakuyesa iwe coombera tirigu catsopano cakuthwa cokhala ndi mano; iwe udzaomba mapiri ndi kuwapera asalale, ndi kusandutsa zitunda mungu.

16 Iwe udzawakupa, ndi mphepo idzawauluza; ndipo kabvumvulu adzawamwaza; ndipo iwe udzasangalala mwa Yehova, udzadzikuza mwa Woyera wa Israyeli,

17 Wosauka ndi wosowa afuna madzi, ndipo palibe, ndi lilume lao lilephera, cifukwa ca ludzu; Ine Yehova ndidzawayankha, Ine Mulungu wa Israyeli sindidzawasiya.

18 Ndidzagwetsa mitsinje pazitunda zoti se, ndi akasupe pakati pa zigwa; ndidzasandutsa cipululu, cikhale thamanda lamadzi, ndi mtunda wouma ukhale magwero a madzi.

19 Ndidzabzala m'cipululu mkungudza, ndi msangu, ndi mcisu, ndi mtengo waazitona; ndidzaika m'cipululu pamodzi mlombwa, ndi mkuyu, ndi naphini;

20 kuti iwo aone ndi kudziwa, ndi kulingalira, ndi kumvetsa pamodzi, kuti dzanja la Yehova lacita ici, ndipo Woyera wa Israyeli wacilenga ici.

21 Onetsani mlandu wanu, ati Yehova; turutsani zifukwa zanu zolimba, ati Mfumu ya Yakobo.

22 Aziturutse, atichulire ife, cimene cidzaoneka; chulani inu zinthu zakale, zinali zotani, kuti ife tiganizire pamenepo, ndi kudziwa mamariziro ao; kapena tionetseni ife zinthu zimene zirinkudza.

23 Chulani zinthu zimene zirinkudza m'tsogolo, kuti ife tidziwe kuti inu ndinu milungu; inde, citani zabwino, kapena citani zoipa, kuti ife tiopsyedwe, ndi kuona pamodzi.

24 Taonani, inu muli acabe, ndi nchito yanu yacabe; wonyansa ali iye amene asankha inu.

25 Ndautsa wina wakucokera kumpoto; ndipo iye wafika wakucokera poturuka dzuwa, amene achula dzina langa; ndipo iye adzafika pa olamulira, monga matope, ndi monga muumbi aponda dothi la mbiya.

26 Ndani wachula ico ciyambire, kuti ife ticidziwe? ndi nthawi zakale, kuti ife tinene, Iye ali wolungama? inde, palibe wina amene achula, inde, palibe wina amene asonyeza, inde, palibe wina amene amvetsa mau anu.

27 Poyamba Ine ndidzati kwa Ziyoni, Taona, taona iwo; ndipo ndidzapereka kwa Yerusalemu wina, amene adza ndi mau abwino.

28 Ndipo pamene ndayang'ana, palibe munthu; ngakhale mwa iwo, palibe phungu, amene angathe kuyankha mau, pamene ndiwafunsa.

29 Taona, iwo onse, nchito zao zikhala zopanda pace ndi zacabe; mafano ao osungunula ndiwo mphepo ndi masokonezo.

42

1 Taona Mtumiki wanga, amene ndimgwiriziza; Wosankhika wanga, amene moyo wanga ukondwera naye; ndaika mzimu wanga pa Iye; Iye adzaturutsira amitundu ciweruziro.

2 Iye sadzapfuula, ngakhale kukuwa, pena kumvetsa mau ace m'khwalala.

3 Bango lophwanyika sadzalityola, ndi lawi lozirala sadzalizima; adzaturutsa ciweruzo m'zoona.

4 Iye sadzalephera kapena kudololoka, kufikira atakhazikitsa ciweruzo m'dziko lapansi; ndipo zisumbu zidzalindira cilamulo cace.

5 Atero Mulungu Yehova, Iye amene analenga thambo, nalifutukula, nayala ponse dziko lapansi, ndi cimene cituruka m'menemo, Iye amene amapatsa anthu a m'menemo mpweya, ndi mzimu kwa iwo amene ayenda m'menemo;

6 Ine Yehova ndakuitana Iwe m'cilungamo, ndipo ndidzagwira dzanja lako ndi kusunga Iwe, ndi kupatsa Iwe ukhale pangano la anthu, ndi kuunika kwa amitundu;

7 kuti utsegule maso akhungu, uturutse am'nsinga m'ndende, ndi iwo amene akhala mumdima, aturuke m'nyumba ya kaidi.

8 Ine ndine Yehova; dzina langa ndi lomweli; ndipo ulemerero wanga Ine sindidzapereka kwa wina, ngakhale kunditamanda kwa mafano osemedwa.

9 Taona, zinthu zakale zaoneka, ndipo zatsopano Ine ndizichula; zisanabuke ndidzakumvetsani.

10 Yimbirani Yehova nyimbo yatsopano, ndi matamando ace kucokera ku malekezero a dziko lapansi; inu amene mutsikira kunyanja, ndi zonse ziri m'menemo, zisumbu ndi okhala mommo.

11 Cipululu ndi midzi yace ikweze mau ao, midzi imene Kedara akhalamo; okhala m'Sela ayimbe, akuwe kucokera pamwamba pa mapiri.

12 Apereke ulemerero kwa Yehova, anene matamando ace m'zisumbu.

13 Yehova adzaturuka ngati munthu wamphamvu; adzautsa nsanje ngati munthu wa nkhondo; Iye adzapfuula, inde adzakuwa zolimba; adzacita zamphamvu pa adani ace.

14 Ndakhala nthawi yambiri wosalankhula; ndakhala cete ndi kudzithungata ndekha; tsopano ndidzapfuula ngati mkazi wobala; ndidzapuma modukizadukiza ndi wefuwefu pamodzi.

15 Ndidzapasula mapiri ndi zitunda, ndi kuumitsa zitsamba zao zonse; ndi kusandutsa nyanja zisumbu, ndi kuumitsa matamanda.

16 Ndipo ndidzayendetsa akhungu m'khwalala, limene iwo salidziwa; m'njira zimene iwo sazidziwa ndidzawatsogolera; ndidzawalitsa mdima m'tsogolo mwao, ndi kulungamitsa malo okhota. Zinthu Izi ine ndidzacita, ndipo sindidzawasiya.

17 Iwo adzabwezedwa m'mbuyo, adzakhala ndi manyazi ambiri amene akhulupirira mafano osemedwa, nati kwa mafano oyengeka, Inu ndinu milungu yathu.

18 Imvani, agonthi inu; yang'anani, akhungu inu, kuti muone.

19 Ndani ali wakhungu, koma mtumiki wanga? pena wagonthi, monga mthenga wanga, amene ndimtumiza? ndani ali wakhungu monga bwenzi langa, ndi wakhungu monga mtumiki wa Yehova?

20 Iwe waona zinthu zambiri, koma susamalira konse; makutu ako ali otseguka, koma sumva konse.

21 Cinakondweretsa Yehova cifukwa ca cilungamo cace kukuza cilamulo, ndi kucilemekeza.

22 Koma awa ndiwo anthu olandidwa zao ndi kufunkhidwa; iwo onse agwa m'mauna, nabisidwa m'nyumba zakaidi; alandidwa zao, palibe wowapulumutsa; afunkhidwa ndipo palibe woti, Bwezerani.

23 Ndani mwa inu adzachera khutu lace pamenepo? amene adzamvera ndi kumva nthawi yakudza?

24 Ndani anapereka Yakobo, kuti afunkhidwe, ndi Israyeli, kuti awawanyidwe? kodi si Yehova? Iye amene tamcimwira, ndi amene iwo anakonda kuyenda m'njira zace, ngakhale kumvera ciphunzitso cace.

25 Cifukwa cace anatsanulira pa iye mkwiyo wace waukali, ndi mphamvu za nkhondo; ndipo unamyatsira moto kuzungulira kwace, koma iye sanadziwa; ndipo unamtentha, koma iye sanacisunga m'mtima.

43

1 Koma tsopano atero Yehova, amene anakulenga iwe Yakobo, ndi Iye amene anakupanga iwe Israyeli, Usaope, cifukwa ndakuombola iwe, ndakuchula dzina lako, iwe uli wanga.

2 Pamene udulitsa pamadzi ndiri pamodzi ndi iwe; ndi pooloka mitsinje sidzakukokolola; pakupyola pamoto sudzapsya; ngakhale lawi silidzakutentha.

3 Cifukwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wako, Woyera wa Israyeli, Mpulumutsi wako; ndapatsa Aigupto dombolo lako, Etiopia ndi Seba m'malo mwako.

4 Pokhala iwe wa mtengo wapatari pamaso panga, ndi wolemekezeka, ndipo ndakukonda iwe; Ine ndidzakuombola ndi anthu, ndi kupereka anthu m'malo mwa moyo wako.

5 Usaope; pakuti Ine ndiri ndi iwe; ndidzatenga mbeu zako kucokera kum'mawa, ndi kusonkhanitsa iwe kucokera kumadzulo.

6 Ine ndidzati ndi kumpoto, Pereka; ndi kumwera, Usaletse; bwera nao ana anga amuna kucokera kutari, ndi ana anga akazi kucokera ku malekezero a dziko lapansi;

7 yense wochedwa dzina langa, amene ndinamlenga cifukwa ca ulemerero wanga; ndinamuumba iye; inde, ndinampanga iye.

8 Turutsani anthu akhungu, amene ali ndi maso, ndi agonthi, amene ali ndi makutu.

9 Amitundu onse asonkhane pamodzi, ndi anthu aunjikane; ndani mwa iwo anganene ici ndi kuonetsa ife zinthu zakale? atenge mboni zao, kuti abvomerezeke ndi olungama; pena amve, nanene zoonadi.

10 Inu ndinu mboni zanga, ati Yehova, ndi mtumiki wanga, amene ndakusankha; kuti mundidziwe, ndi kundikhulupirira Ine, ndi kuzindikira, kuti Ine ndine; ndisanakhale Ine, panalibe Mulungu wolengedwa, ngakhale pambuyo panga sipadzakhala wina.

11 Ine, Inetu ndine Yehova; ndipo palibe Mpulumutsi, koma Ine ndekha.

12 Ine ndalalikira, ndipo ndikupulumutsa ndi kumvetsa, ndipo panalibe Mulungu wacilendo pakati pa inu; cifukwa cace inu ndinu mboni zanga, ati Yehova, ndipo Ine ndine Mulungu.

13 Inde ciyambire nthawi Ine ndine, ndipo palibe wina wopulumutsa m'dzanja langa; ndidzagwira nchito, ndipo ndani adzaletsa?

14 Atero Yehova, Mombolo wanu, Woyera wa Israyeli: Cifukwa ca inu ndatumiza ku Babulo, ndipo ndidzatsitsira iwo onse monga othawa, ngakhale Akasidi m'ngalawa za kukondwa kwao.

15 Ine ndine Yehova Woyera wanu, Mlengi wa Israyeli, Mfumu yanu,

16 Atero Yehova, amene akonza njira panyanja, ndi popita m'madzi amphamvu;

17 amene aturutsa gareta ndi ka valo, nkhondo ndi mphamvu; iwo agona pansi pamodzi sadzaukai; iwo atha, azimidwa ngati lawi.

18 Musakumbukire zidapitazo, ngakhale kulingalira zinthu zakale.

19 Taonani, ine ndidzacita cinthu catsopano; tsopano cidzaoneka; kodi simudzacidziwa? Ndidzakonzadi njira m'cipululu, ndi mitsinje m'zidalala.

20 Nyama za m'thengo zidzandilemekeza, ankhandwe ndi nthiwatiwa; cifukwa ndipatsa madzi m'cipululu, ndi mitsinje m'mkhwangwala, ndimwetse anthu anga osankhika;

21 anthu amene ndinadzilengera ndekha, kuti aonetse matamando anga.

22 Komabe iwe sunandiitane Ine, Yakobo; koma iwe walema ndi Ine, Israyeli.

23 Iwe sunanditengere Ine zoweta zazing'ono za nsembe zopsereza zako; kapena kundilemekeza ndi nsembe zako. Sindinakutumikiritsa ndi nsembe zaufa, kapena kukutopetsa ndi zonunkhira.

24 Iwe sunandigulire Ine nzimbe ndi ndarama, pena kundikhutitsa ndi mafuta a nsembe zako. Koma iwe wanditumikiritsa ndi macimo ako, wanditopetsa ndi mphulupulu zako.

25 Ine, Inedi, ndine amene ndifafaniza zolakwa zako, cifukwa ca Ine mwini; ndipo Ine sindidzakumbukira macimo ako.

26 Undikumbutse Ine; tiyeni, tinenane pamodzi; fotokoza mlandu wako, kuti ukalungamitsidwe.

27 Atate wako woyamba anacimwa, ndi otanthauzira ako andilakwira Ine.

28 Cifukwa cace ndidzaipitsa akuru a kacisi, ndipo ndidzasanduliza Yakobo akhale temberero, ndi Israyeli akhale citonzo.

44

1 Koma tsopano, imva Yakobo, mtumiki wanga, ndi Israyeli, amene ndakusankha;

2 atero Yehova, amene anakutenga iwe, nakuumba kucokera m'mimba, amene adzathangata iwe. Usaope Yakobo, mtumiki wanga ndi iwe, Yesuruni, amene ndakusankha iwe.

3 Pakuti ndidzathira madzi pa dziko limene liribe madzi, ndi mitsinje pa nthaka youma; ndidzathira mzimu wanga pa mbeu yako, ndi mdalitso wanga pa obadwa ako;

4 ndipo iwo adzaphuka pakati pa maudzu, ngati msondodzi m'mphepete mwa madzi.

5 Wina adzati, Ine ndiri wa Yehova; ndi wina adzadzicha yekha ndi dzina la Yakobo, ndipo wina adzalemba ndi dzanja lace, Ndine wa Yehova, ndi kudzicha yekha ndi mfunda wa lsrayeli.

6 Atero Yehova, Mfumu ya Israyeli ndi Mombolo wace, Yehova wa makamu, Ine ndiri woyamba ndi womariza, ndi popanda Ine palibenso Mulungu.

7 Ndipo ndani adzaitana monga Ine, ndi kulalikira ici ndi kundilongosolera ici, cikhazikitsire Ine anthu akale? milunguyo iwadziwitse zomwe zirinkudza, ndi za m'tsogolo.

8 Musaope inu, musakhale ndi mantha; kodi ndinanena kwa iwe zakale, ndi kuzionetsa zimenezo, ndipo inu ndinu mboni zanga. Kodi popanda Ine aliponso Mulungu? Iai, palibe thanthwe; sindidziwa liri lonse.

9 Omwe apanga fano losema onsewo asokonezeka; ndipo zokondweretsa zao sadzapindula nazo kanthu; ndipo mboni zao siziona, kapena kudziwa; kuti akhale ndi manyazi.

10 Ndani wapanga mulungu, kapena kusungunula fano losema losapindula kanthu?

11 Taonani anzace onse adzakhala ndi manyazi, ndi amisiri ace ndi anthu; asonkhane onse pamodzi, aimirire; adzaopa, iwo onse adzakhala ndi manyazi.

12 Wacipala acita zace ndi nsompho, nagwira nchito ndi makala, nafanizira fanolo ndi nyundo, nagwira nchito yace ndi mkono wace wamphamvu; inde, ali ndi njala, ndipo mphamvu zace zilephera; iye samwa madzi, nalefuka.

13 Mmisiri wa mitengo atambalitsa cingwe; nalilemba ndi colembera, nalikonza ndi ncerero, nalilemba ndi zolinganizira, nalifanizira monga maonekedwe a munthu, monga munthu wokongola, kuti likhale m'nyumba.

14 Iye adzidulira yekha mikungudza, natenga mtengo wambawa, ndi wathundu, ndi kudzisankhira yekha wina wa mitengo ya nkhalango; naoka mtengo wamlombwa, mvula niukulitsa.

15 Ndipo udzakhala kuti munthu autenthe; iye natengako, nauotha moto; inde auyatsa, naoca mkate; inde, apanga mlungu, naulambira, naupanga fano losema, naligwadira.

16 Iye atenthako mbali yina pamoto; ndi mbali yinayo adya nyama; akazinga zokazinga, nakhuta, inde, aotha moto, nati, Ha, ndakongonoka, ndauona moto.

17 Ndipo cotsalaco apanga mlungu, ngakhale fano lace losema; iye aligwadira, nalipembedza, nalipemphera nati, Ndipulumutse ine, cifukwa kuti ndinu mulungu wanga.

18 Iwo sadziwa, kapena kuzindikira, cifukwa pamaso pao papakidwa thope, kuti sangaone, ndi m'mitima mwao kuti sangadziwitse.

19 Palibe wina wokumbukira, kapena kudziwa, kapena kuzindikira, ndi kuti, Ndatentha mbali yina pamoto, inde ndaocanso mkate pamakala pace, ndakazinga nyama ndi kuidya; kodi ndicipange cotsala cace, cikhale conyansa? ndidzagwadira kodi tsinde la mtengo?

20 Iye adya phulusa; mtima wodzinyenga wampambutsa, kuti iye sangapulumutse moyo wace, pena kunena, Kodi simuli kunama m'dzanja langa lamanja?

21 Kumbukira zinthu izi, Yakobo; ndi Israyeli, pakuti iwe ndiwe mtumiki wanga; ndakuumba, iwe ndiwe mtumiki wanga, Israyeli, sindidzakuiwala.

22 Ine ndafafaniza monga mtambo wocindikira zolakwa zako, ndi monga mtambo macimo ako; bwerera kwa Ine, pakuti ndakuombola.

23 Yimbani m'mwamba inu, pakuti Yehova wacicita ico; kuwani inu, mbali za pansi pa dziko; yimbani mapiri inu; nkhalango iwe, ndi mitengo yonse m'menemo; cifukwa kuti Yehova wapulumutsa Yakobo, ndipo adzadzilemekezetsa yekha mwa Israyeli.

24 Atero Yehova, Mombolo wako, ndi Iye amene anakuumba iwe m'mimba, Ine ndine Yehova, amene ndipanga zinthu zonse, ndi kufunyulula ndekha zakumwamba, ndi kuyala dziko lopansi; ndani ali ndi Ine?

25 Ndine amene nditsutsa zizindikilo za matukutuku, ndi kucititsa misala oombeza ula; ndi kubwezera m'mbuyo anthu anzeru, ndi kupusitsa nzeru zao:

26 Ndine amene ndilimbitsa mau a mtumiki wanga, kucita uphungu wa amithenga anga; ndi kunena za Yerusalemu, Adzakhalamo anthu; ndi za midzi ya Yuda; Idzamangidwa; ndipo ndidzautsa malo abwinja ace.

27 Ndine amene nditi kwa nyanja yakuya, Iphwa, ndipo ndidzaumitsa nyanja zako;

28 ndi kunena za Koresi, Iye ndiye mbusa wanga, ndipo adzacita zofuna zanga zonse; ndi kunena za Yerusalemu, Adzamangidwa; ndi kwa Kacisi, Maziko ako adzaikidwa.

45

1 Atero Yehova kwa wodzozedwa wace kwa Koresi, amene dzanja lace lamanja ndaligwiritsa, kuti agonjetse mitundu ya anthu pamaso pace, ndipo ndidzamasula m'cuuno mwa mafumu; atsegule zitseko pamaso pace, ndi zipata sizidzatsekedwa:

2 Ndidzakutsogolera ndi kusalaza pokakala; ndidzatyolatyola zitseko zamkuwa, ndi kudula pakati akapici acitsulo;

3 ndipo ndidzakupatsa iwe cuma ca mumdima, ndi zolemera zobisika za m'malo am'tseri, kuti iwe udziwe kuti Ine ndine Yehova, amene ndikuitana iwe dzina lako, ndine Mulungu wa Israyeli.

4 Ndakuitana iwe dzina lako, cifukwa ca Yakobo mtumiki wanga ndi Israyeli wosankhidwa wanga; ndakuonjezera dzina, ngakhale iwe sunandidziwa Ine.

5 Ine ndiri Yehova, ndipo palibe winanso; popanda Ine palibe Mulungu; ndidzakumanga m'cuuno, ngakhale sunandidziwa;

6 kuti anthu akadziwe kucokera ku maturukiro a dzuwa ndi kumadzulo, kuti palibe wina popanda Ine; Ine ndine Yehova, palibe winanso.

7 Ine ndilenga kuyera ndi mdima, Ine ndilenga mtendere ndi coipa, Ine ndine Yehova wocita zinthu zonse zimenezi.

8 Igwani pansi, inu m'mwamba, kucokera kumwamba, thambo litsanulire pansi cilungamo; dziko lapansi litseguke, kuti libalitse cipulumutso, nilimeretse cilungamo cimere pamodzi; Ine Yehova ndinacilenga cimeneco.

9 Tsoka kwa iye amene akangana ndi Mlengi wace! phale mwa mapale a dziko lapansi! Kodi dongo linganene kwa iye amene aliumba, Kodi upanga ciani? pena nchito yako, Iye alibe manja?

10 Tsoka kwa iye amene ati kwa atate wace, Kodi iwe ubalanji? pena kwa mkazi, Ulikusauka ninji iwe?

11 Atero Yehova Woyera wa Israyeli ndi Mlengi wace, Ndifunse Ine za zinthu zimene zirinkudza; za ana anga amuna, ndi za nchito ya manja anga, ndilamulireni Ine.

12 Ine ndalenga dziko lapansi, ndalengamo munthu; Ine, ngakhale manja anga, ndafunyulula kumwamba, ndi zonse za m'menemo, ndinazilamulira ndine.

13 Ine ndautsa Koresi m'cilungamo, ndipo ndidzalungamitsa njira zace zonse; iye adzamanga mudzi wanga, nadzaleka andende anga anke mwa ufulu, wosati ndi mtengo pena mphotho, ati Yehova wa makamu.

14 Atero Yehova, Nchito ya Aigupto, ndi malonda a Kusi, ndi a Sabea, amuna amsinkhu adzakugonjera, nadzakhala ako; nadzakutsata pambuyo m'maunyolo; adzakugonjera, nadzakugwira; adzakupembedza ndi kunena, Zoona Mulungu ali mwa iwe; ndipo palibenso wina, palibe Mulungu.

15 Ndithu Inu ndinu Mulungu, amene mudzibisa nokha, Mulungu wa Israyeli, Mpulumutsi.

16 Iwo adzakhala ndi manyazi, inde, adzathedwa nzeru onsewo; adzalowa m'masokonezo pamodzi, amene apanga mafano.

17 Koma Israyeli adzapulumutsidwa ndi Yehova ndi cipulumutso cosatha; inu simudzakhala ndi manyazi, pena kuthedwa nzeru ku nthawi zosatha.

18 Pakuti atero Yehova amene analenga kumwamba, Iye ndiye Mulungu amene anaumba dziko lapansi, nalipanga; Iye analikhazikitsa, sanalilenga mwacabe; Iye analiumba akhalemo anthu; Ine ndine Yehova; ndipo palibenso wina.

19 Ine sindinanena m'tseri m'malo a dziko la mdima; Ine sindinati kwa mbeu ya Yakobo, Mundifune Ine mwacabe; Ine Yehova ndinena cilungamo, ndinena zimene ziri zoona.

20 Sonkhanani nokha, mudze; yandikirani cifupi pamodzi, inu amene mwapulumuka amitundu; iwo alibe nzeru, amene anyamula mtengo wa fano lao losema, ndi kupemphera mlungu wosakhoza kupulumutsa.

21 Nenani inu, turutsani mlandu wanu; inde, acite uphungu pamodzi; ndani waonetsa ici ciyambire nthawi yakale? ndani wanena ici kale? kodi si ndine Yehova? ndipo palibenso Mulungu wina popanda Ine; Mulungu wolungama, ndi Mpulumutsi; palibenso wina popanda Ine.

22 Yang'anani kwa Ine, mupulumutsidwe, inu malekezero onse a dziko; pakuti Ine ndine Mulungu, palibe wina.

23 Ndadzilumbira ndekha, mau acokera m'kamwa mwanga m'cilungamo, ndipo sadzabwerera, kuti mabondo onse adzandigwadira Ine, malilime onse nadzalumbira Ine.

24 Koma mwa Yehova yekha, wina adzati kwa Ine, muli cilungamo ndi mphamvu; ngakhale kwa Iyeyo anthu adzafika, ndi onse amene anamkwiyira, adzakhala ndi manyazi.

25 Mwa Yehova mbeu yonse ya Israyeli idzalungamitsidwa ndi 7 kudzikuza.

46

1 Beli agwada pansi, Nebo awerama; mafano ao ali pa zoweta, ndi pa ng'ombe; zinthu zimene inu munanyamula ponseponse ziyesedwa mtolo, katundu wakulemetsa nyama.

2 Milunguyo iwerama, igwada pansi pamodzi; singapulumutse katundu, koma iyo yeni yalowa m'ndende.

3 Mverani Ine, banja la Yakobo, ndi otsala onse a banja la Israyeli, amene ndakunyamulani kuyambira m'mimba, ndi kukusenzani cibadwire;

4 ngakhale mpaka mudzakalamba Ine ndine, ndipo ngakhale mpaka tsitsi laimvi, Ine ndidzakusenzani inu; ndalenga, ndipo ndidzanyamula; inde, ndidzasenza, ndipo ndidzapulumutsa.

5 Kodi mudzandifanizira ndi yani, ndi kundilinganiza ndi kundiyerekeza, kuti ife tifanane?

6 Amene ataya golidi, namturutsa m'thumba, ndi kuyesa siliva ndi muyeso, iwo alemba wosula golidi; iye napanga nazo mlungu; iwo agwada pansi, inde alambira.

7 Iwo amanyamula mlunguwu paphewa, nausenza, naukhazika m'malo mwace, nukhala ciriri; pamalo pacepo sudzasunthika; inde, wina adzaupfuulira, koma sungathe kuyankha, kapena kumpulumutsa m'zobvuta zace.

8 Kumbukirani ici, nimucirimike, mudzikumbutsenso, olakwa inu.

9 Kumbukirani zinthu zoyamba zakale, kuti Ine ndine Mulungu, ndipo palibenso wina; Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina wofana ndi Ine;

10 ndilalikira za cimariziro kuyambira paciyambi, ndi kuyambira nthawi zakale ndinena zinthu zimene zisanacitidwe; ndi kunena, Uphungu wanga udzakhala, ndipo ndidzacita zofuna zanga zonse;

11 ndiitana mbalame yolusa kucokera kum'mawa, ndiye munthu wa uphungu wanga, kucokera ku dziko lakutari; inde, ndanena, ndidzacionetsa; ndinatsimikiza mtima, ndidzacicitanso.

12 Mverani Ine, inu olimba mtima, amene muli kutari ndi cilungamo;

13 ndiyandikizitsa cifupi cilungamo canga sicidzakhala patari, ndipo cipulumutso canga sicidzacedwa; ndipo ndidzaika cipulumutso m'Ziyoni, ca kwa Israyeli ulemerero wanga.

47

1 Tsika, ukhale m'pfumbi, namwaliwe, mwana wamkazi wa Babulo; khala pansi popanda mpando wacifumu, mwana wamkazi wa Akasidi, pakuti iwe sudzayesedwanso wozizira ndi wololopoka.

2 Tenga mipero, nupere ufa; cotsa cophimba cako, bvula copfunda, kwinda m'mwendo, oloka mitsinje.

3 Marisece ako adzakhala osapfundidwa, inde, manyazi ako adzaoneka; ndidzacita kubwezera, osasamalira munthu.

4 Mombolo wathu, Yehova wa makamu ndi dzina lace, Woyera wa Israyeli.

5 Khala iwe cete, lowa mumdima, mwana wamkazi wa Akasidi; pakuti sudzachedwanso mkazi wa maufumu.

6 Ndinakwiyira anthu anga, ndinaipitsa colowa canga, ndi kuwapereka m'manja ako; koma iwe sunawaonetsera cifundo; wasenzetsa okalamba goli lako lolemera ndithu.

7 Ndipo unati, Ndidzakhala mkazi wa mfumu wa nthawi zonse; ndipo sunasamalira izi mumtima mwako, kapena kukumbukira comarizira cace.

8 Cifukwa cace tsono, imva ici, iwe wotsata zokondweretsa, amene umakhala mosatekeseka, amene umati mumtima mwako, Ine ndine, ndipo popanda ine palibenso wina; sindidzakhala monga mkazi wamasiye, kapena kudziwa kumwalira kwa ana;

9 koma izi ziwiri zidzakugwera mwadzidzidzi, tsiku limodzi kumwalira kwa ana ndi umasiye zidzakugwera; mokwanira monse, pakati pa unyinji wa matsenga ako, ndi pakati pa maphenda ako ambirimbiri.

10 Pakuti wakhulupirira zoipa zako, wati, Palibe wondiona ine; nzeru zako ndi cidziwitso cako zakusandutsa woipa; ndipo wanena mumtima mwako, Ndine, ndipo popanda ine palibenso wina.

11 Cifukwa cace coipa cidzafika pa iwe; sudzadziwa kuca kwace, ndipo cionongeko cidzakugwera; sudzatha kucikankhira kumbali; ndipo cipasuko cosacidziwa iwe cidzakugwera mwadzidzidzi.

12 Taima tsopano ndi maphendo ako, ndi unyinji wa matsenga ako, m'menemo iwe unagwira nchito ciyambire ubwana wako; kuti kapena udzatha kupindula, kuti kapena udzapambana.

13 Watopa mu uphungu wako wambiri; aimirire tsopano openda zam'mwamba, oyang'ana nyenyezi, akuneneratu mwezi ndi mwezi, ndi kukupulumutsa pa zinthu zimene zidzakugwera.

14 Taona, iwo adzakhala ngati ziputu, moto udzawatentha iwo; sadzadzipulumutsa okha ku mphamvu za malawi; motowo sudzakhala khala loothako, pena moto wakukhalako.

15 Zinthu zomwe unagwira nchito yace, zidzatero nawe; iwo amene anacita malonda ndi iwe ciyambire pa ubwana wako, adzayenda yense kunka kumalo kwace; sipadzakhala wopulumutsa iwe.

48

1 Imvani inu ici, banja la Yakobo, amene muchedwa ndi dzina la Israyeli, amene munaturuka m'madzi a Yuda amene mulumbira dzina la Yehova ndi kuchula dzina la Mulungu wa Israyeli, koma si m'zoona, pena m'cilungamo.

2 Pakuti adziyesa okha a mudzi wopatulika, ndi kudzikhazikitsa iwo okha pa Mulungu wa Israyeli; dzina lace ndi Yehova wa makamu.

3 Ndanena zinthu zoyamba kuyambira kale; inde, izo zinaturuka m'kamwa mwanga, ndipo ndinazisonyeza; mwadzidzidzi ndinazicita izo, ndipo zinaoneka.

4 Popeza ndinadziwa, kuti uli wokanika, ndi khosi lako liri mtsempha wacitsulo, ndi mphumi yako mkuwa;

5 cifukwa cace ndinakudziwitsa ici kuyambira kale; cisanaoneke ndinakusonyeza ico, kuti iwe unganene, Fano langa lacita izo, ndi cifanizito canga cosema, ndi cifaniziro canga coyenga zinazilamulira.

6 Iwe wacimva taona zonsezi; ndipo inu kodi inu simudzacinena? Ndakusonyeza iwe zinthu zatsopano kucokera nthawi yino, ngakhale zinthu zobisika, zimene iwe sunazidziwe.

7 Zalengedwa tsopano, zosati kuyambira kale; ndipo lisanafike tsiku laleroli iwe sunazimve; unganene, Taonani, ndinazidziwa.

8 Inde, iwe sunamva; inde, sunadziwe; inde, kuyambira kale khutu lako silinatsegudwe; pakuti ndinadziwa kuti iwe wacita mwaciwembu ndithu, ndipo unayesedwa wolakwa cibadwire.

9 Cifukwa ca dzina langa ndidzacedwetsa mkwiyo wanga, ndi cifukwa ca kutamanda kwanga ndidzakulekerera, kuti ndisakucotse.

10 Taona ndakuyenga, koma si monga siliva, ndakuyesa iwe m'ng'anjo ya masautso.

11 Cifukwa ca Ine ndekha, cifukwa ca Ine ndekha ndidzacita ici, pakuti dzina langa lidetsedwerenji? ndi ulemerero wanga sindidzaupereka kwa wina.

12 Mverani Ine, Yakobo ndi Israyeli, oitanidwa anga, Ine ndine; ndine woyamba, Inenso ndine womariza.

13 Inde dzanja langa linakhazika maziko a dziko lapansi, ndi dzanja langa lamanja linafunyulula m'mwamba; pakuziitana Ine ziimirira pamodzi.

14 Sonkhanani inu nonse ndi kumva, ndani mwa iwo aonetsa zinthu izi? Iye amene Yehova anamkonda, iye adzacita kufuna kwace pa Babulo, ndi mkono wace udzakhala pa Akasidi.

15 Ine, ngakhale Ine ndanena; inde ndamwitana iye, ndamfikitsa, ndipo adzapindula nayo njira yace.

16 Idzani inu cifupi ndi Ine, imvani ici; kuyambira pa ciyambi sindinanene m'tseri; ciyambire zimenezi, Ine ndiripo; ndipo tsopano Ambuye Mulungu wanditumiza Ine ndi mzimu wace.

17 Atero Yehova, Mombolo wako, Woyera wa Israyeli, Ine ndine Yehova, Mulungu wako, amene ndikuphunzitsa kupindula, amene ndikutsogolera m'njira yoyenera iwe kupitamo.

18 Mwenzi utamvera malamulo anga mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje, ndi cilungamo cako monga mafunde a nyanja;

19 mbeu yakonso ikadakhala monga mcenga ndi obadwa a m'cuuno mwako momwemo; dzina lace silikadacotsedwa, pena kuonongeka pamaso panga.

20 Turukani inu m'Babulo, athaweni Akasidi; ndi mau akuyimba nenani inu, bukitsani ici, lalikirani ici, ngakhale ku malekezero a dziko; nenani, Yehova waombola mtumiki wace Yakobo.

21 Ndipo iwo sanamva ludzu, pamene Iye anawatsogolera m'mapululu; anawaturutsira madzi kuturuka m'matanthwe; anadulanso thanthwe, madzi nabulika.

22 1 Kulibe mtendere, ati Yehova, kwa oipa.

49

1 Mverani Ine, zisumbu inu, mumvere anthu inu akutari; Yehova anandiitana Ine ndisanabadwe; m'mimba mwa amai Iye anachula dzina langa;

2 nacititsa pakamwa panga ngati lupanga lakuthwa, mu mthunzi wa dzanja lace wandibisa Ine; wandipanga Ine mubvi wotuulidwa; m'phodo mwace Iye wandisungitsa Ine, nati kwa Ine,

3 Iwe ndiwe mtumiki wanga, Israyeli, amene ndidzalemekezedwa nawe.

4 Koma ndinati, Ndagwira nchito mwacabe, ndatha mphamvu zanga pacabe, ndi mopanda pace; koma ndithu ciweruziro canga ciri ndi Yehova, ndi kubwezera kwanga kuli ndi Mulungu wanga.

5 Ndipo tsopano, ati Yehova, amene anandiumba Ine ndisanabadwe ndikhale mtumiki wace, kubwezanso Yakobo kwa Iye, ndi kuti Israyeli asonkhanidwe kwa Iye; cifukwa Ine ndiri wolemekezeka pamaso pa Yehova, ndipo Mulungu wanga wakhala mphamvu zanga;

6 inde, ati, Ciri cinthu copepuka ndithu kuti Iwe ukhale mtumiki wanga wakuutsa mafuko a Yakobo, ndi kubwezera osungika a Israyeli; ndidzakupatsanso ukhale kuunika kwa amitundu, kuti ukhale cipulumutso canga mpaka ku malekezero a dziko lapansi.

7 Atero Yehova, Mombolo wa Israyeli, ndi Woyera wace, kwa Iye amene anthu amnyoza, kwa Iye amene mtundu wathu unyansidwa naye, kwa mtumiki wa olamulira: Mafumu adzaona, nadzauka; akalonga nadzalambira cifukwa ca Yehova, amene ali wokhulupirika, ngakhale Woyera wa Israyeli, amene anakusankha Iwe.

8 Atero Yehova, Nthawi yondikomera ndakuyankha Iwe, ndi tsiku la cipulumutso ndakuthandiza; ndipo ndidzakusunga ndi kupatsa Iwe ukhale pangano la anthu, kuti ukhazikitse dziko, nuwalowetse m'zolowa zopasuka m'malo abwinja;

9 ndi kunena kwa iwo amene ali omangidwa, Mukani, kwa iwo amene ali mumdima, Dzionetseni nokha. Iwo adzadya m'njira, ndi m'zitunda zonse zoti se mudzakhala busa lao.

10 Iwo sadzakhala ndi njala, pena ludzu; ngakhale thukuta, pena dzuwa silidzawatentha; pakuti Iye amene wawacitira cifundo, adzawatsogolera, ngakhale pa akasupe a madzi adzawatsogolera.

11 Ndipo ndidzasandutsa mapiri anga onse akhale njira, ndipo makwalala anga adzakwezeka.

12 Taonani, awa adzacokera kutari; ndipo taonani, awa ocokera kumpoto, ndi kumadzulo; ndi awa ocokera ku dziko la Sinimu.

13 Yimbani inu, m'mwamba, nukondwere iwe dziko lapansi, yimbani inu mapiri, pakuti Yehova watonthoza mtima wa anthu ace, nadzacitira cifundo obvutidwa ace.

14 Koma Ziyoni anati, Yehova wandisiya ine, ndipo Ambuye wandiiwala ine.

15 Kodi mkazi angaiwale mwana wace wa pabere, kuti iye sangacitire cifundo mwana wombala iye? inde awa angaiwale, koma Ine sindingaiwale iwe.

16 Taona ndakulembera iwe pa zikhato za manja anga; makoma ako alipo masiku onse pamaso panga,

17 Ana ako afulumira; opasula ako ndi iwo amene anakusakaza adzacoka pa iwe.

18 Tukula maso ako kuunguza-unguza, nuone; onsewa asonkhana pamodzi, nadza kwa iwe. Pali Ine, ati Yehova, iwe ndithu udzadzibveka wekha ndi iwo onse, monga ndi cokometsera, ndi kudzimangira nao m'cuuno ngati mkwatibwi.

19 Pakuti, kunena za tnalo ako osiyidwa ndi abwinja ndi dziko lako limene lapasulidwa tsopano, ndithu iwe udzakhala wocepera okhalamo, ndi iwo amene anakumeza iwe adzakhala kutari.

20 Ana ako amasiye adzanena m'makutu ako, Malo andicepera ine, ndipatse malo, kuti ndikhalemo.

21 Pamenepo udzati m'mtima mwako, Ndani wandibalitsa ine amenewa, popeza ana anga anacotsedwa kwa ine, ndipo ndiri wouma, ndi wocotsedwa m'dziko, ndi woyendayenda kwina ndi kwina? ndipo ndani wadza ndi awa? Taona ndinasiyidwa ndekha, amenewa anali kuti?

22 Atero Ambuye Yehova, Taona ndidzakodola anthu a mitundu, ndi kukwezera anthu mbendera yanga; ndipo adzabwera nao ana ako amuna pa cifuwa cao, ndi ana ako akazi adzatengedwa pa mapewa ao.

23 Ndipo mafumu adzakulera, ndi akazi ao akuru adzakuyamwitsa; iwo adzakugwadira ndi nkhope zao zoyang'ana pansi, nadzaseteka pfumbi la m'mapazi ako: ndipo iwe udzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndi iwo amene alindira Ine sadzakhala ndi manyazi.

24 Kodi cofunkha cingalandidwe kwa wamphamvu, pena am'nsinga a woopsya angapulumutsidwe?

25 Koma atero Yehova, Ngakhale am'nsinga a wamphamvu adzalandidwa, ndi cofunkha ca woopsya cidzapulumutsidwa; pakuti Ine ndidzakangana naye amene akangana ndi iwe, ndipo ndidzapulumutsa ana ako.

26 Ndipo ndidzadyetsa iwo amene atsendereza iwe ndi nyama yao yao; ndi mwazi wao wao; iwo adzaledzera monga ndi vinyo wotsekemera; anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova ndiri Mpulumutsi wako, ndi Mombolo wako, Wamphamvu wa Yakobo.

50

1 Atero Yehova, Kalata wa cilekaniro ca amako ali kuti amene ndinamsudzula naye? pena ndani wa angongole anga amene ndamgulitsa iwe? Taona cifukwa ca zoipa zanu munagulitsidwa, ndi cifukwa ca kulakwa kwanu amanu anacotsedwa.

2 Cifukwa canji ndinafika osapeza munthu? ndi kuitana koma panalibe wina woyankha? Kodi dzanja langa lafupika konse, kuti silingathe kuombola? pena Ine kodi ndilibe mphamvu zakupulumutsa? Taona pa kudzudzula kwanga ndiumitsa nyanja yaikuru, ndi kusandutsa mitsinje cipululu; nsomba zace zinunkha cifukwa mulibe madzi, nizifa ndi ludzu.

3 Ndibveka thambo ndi kuda, ndi kuyesa ciguduli copfunda cace.

4 Ambuye Yehova wandipatsa Ine lilime la ophunzira, kuti ndidziwe kunena mau akucirikiza iye amene ali wolema. Iye andigalamutsa m'mawa ndi im'mawa, nagalamutsa khutu langa kuti limve monga ophunzira.

5 Ambuye Yehova watsegula khutu langa, ndipo sindinakhala wopanduka ngakhale kubwerera m'mbuyo.

6 Ndinapereka msana wanga kwa omenya, ndi masaya anga kwa iwo amene anakudzula tsitsi langa; sindinabisira nkhope yanga manyazi ndi kulabvulidwa.

7 Pakuti Ambuye Yehova adzandithangata Ine; cifukwa cace sindinasokonezedwa; cifukwa cace ndakhazika nkhope yanga ngati mwala, ndipo ndidziwa kuti sindidzakhala ndi manyazi.

8 Iye ali pafupi amene alungamitsa Ine; ndani adzakangana ndi Ine? tiyeni tiimirire tonse pamodzi; mdani wanga ndani? andiyandikire.

9 Taonani, Ambuye Yehova adzathandiza Ine; ndani amene adzanditsutsa? taonani, iwo onse adzatha ngati cobvala, njenjete zidzawadya.

10 Ndani ali mwa inu amene amaopa Yehova, amene amamvera mau a mtumiki wace? Iye amene ayenda mumdima, ndipo alibe kuunika, akhulupirire dzina la Yehova, ndi kutsamira Mulungu wace.

11 Taonani, inu nonse amene muyatsa moto, amene mudzimangira m'cuuno ndi nsakali, yendani inu m'cirangati ca moto wanu, ndi pakati pa nsakali zimene mwaziyatsa. Ici mudzakhala naco ca pa dzanja langa; mudzagona pansi ndi cisoni.

51

1 Mverani Ine, inu amene mutsata cilungamo, inu amene mufuna Yehova; yang'anani ikuthanthwe, kumene inu munasemedwamo, ndi kuuna kwa dzenje, kumene inu munakumbidwamo.

2 Yang'anani kwa Abrahamu kholo lanu, ndi kwa Sara amene anakubalani inu; pakuti pamene iye anali mmodzi yekha ndinamuitana iye; ndipo ndinamdalitsa ndi kumcurukitsa.

3 Pakuti Yehova watonthoza mtima wa Ziyoni, watonthoza mtima wa malo ace onse abwinja; ndipo wasandutsa cipululu cace ngati Edene, ndi nkhwangwara yace ngati munda wa Yehova; kukondwa ndi kusangalala kudzapezedwa m'menemo, mayamikiro, ndi mau a nyimbo yokoma.

4 Mverani Ine, inu anthu anga, ndi kundicherera makutu, iwe, mtundu wa anthu anga; pakuti lamulo lidzacokera kwa ine, ndipo ndidzakhazikitsa ciweruziro canga cikhale kuunika kwa anthu.

5 Cilungamo canga ciripafupi, cipulumutso canga camuka; ndipo mikono yanga idzaweruza anthu; zisumbu zidzandilindira, ndipo adzakhulupirira mkono wanga.

6 Tukulani maso anu kumwamba, ndipo muyang'ane pansi pa dziko; pakuti kumwamba kudzacoka ngati utsi, ndi dziko lidzatha ngati copfunda, ndipo iwo amene akhala m'menemo adzafa cimodzimodzi; koma cipulumutso canga cidzakhala ku nthawi lonse, ndi cilungamo canga sicidzacotsedwa.

7 Mverani Ine, inu amene mudziwa cilungamo, anthu amene mumtima mwao muli lamulo langa; musaope citonzo ca anthu, ngakhale kuopsedwa ndi kutukwana kwao.

8 Pakuti njenjete idzawadya ngati copfunda, ndi mbozi zidzawadya ngati ubweya; koma cilungamo canga cidzakhala ku nthawi zonse, ndi cipulumutso canga ku mibadwo yonse.

9 Galamuka, galamuka, khala ndi mphamvu, mkono wa Yehova; galamuka monga masiku akale, mibadwo ya nthawi zakale. Kodi si ndiwe amene unadula Rahabu zipinjiri zipinjiri, amene unapyoza cinjoka cija?

10 Kodi si ndiwe amene unaumitsa nyanja, madzi akuya kwambiri; amene anasandutsa nyanja zikhale njira ya kupitapo oomboledwa?

11 Ndipo oomboledwa a Yehova adzabwera, nadzafika ku Ziyoni; ndi nyimbo ndi kukondwa kosatha kudzakhala pa mitu yao; adzakhala m'kusangalala ndi kukondwa, ndipo cisoni ndi kuusa moyo kudzacoka.

12 Ine, Inedi, ndine amene nditonthoza mtima wako; kodi iwe ndani, kuti uopa munthu amene adzafa, ndi mwana wa munthu amene adzakhala ngati udzu;

13 waiwala Yehova Mlengi wako, amene anayala m'mwamba, nakhazika maziko a dziko lapansi, ndi kuopabe tsiku lonse cifukwa ca ukali wa wotsendereza, pamene iye akonzeratu kupasula? uli kuti ukali wa wotsendereza?

14 Wam'nsinga wowerama adzamasulidwa posacedwa; sadzafa ndi kutsikira kudzenje, cakudya cace sicidzasowa.

15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wako, amene ndiutsa nyanja, kuti mafunde ace akokome; Yehova wa makamu ndi dzina lace.

16 Ndipo ndaika mau anga m'kamwa mwako; ndipo ndakuphimba ndi mthunzi wa dzanja langa, kuti ndikhazike kumwamba ndi kuika maziko a dziko lapansi, ndi kunena kwa Ziyoni, Inu ndinu anthu anga.

17 Galamuka, galamuka, imirira Yerusalemu amene unamwa m'dzanja la Yehova cikho ca ukali wace; iwe wamwa mbale ya cikho conjenjemeretsa ndi kucigugudiza.

18 Palibenso wina wakumtsogolera mwa ana amuna onse, amene iye anawabala; palibe wina amgwira dzanja mwa ana onse anawalera.

19 Izi ziwiri zakugwera; ndani adzakulira iwe? bwinja ndi cipasuko, njala ndi lupanga; ndidzatonthoza mtima wako bwanji?

20 Ana ako amuna akomoka; agona pamtu pa makwalala onse, monga nswala muukonde; adzala ndi ukali wa Yehova, kudzudzula kwa Mulungu wako,

21 Cifukwa cace imva ici tsopano, iwe wobvutidwa ndi woledzera koma si ndi vinyo ai;

22 atero Ambuye ako Yehova, ndi Mulungu wako amene anena mlandu wa anthu ace, Taona, ndacotsa m'dzanja mwako cikho conjenjemeretsa, ngakhale mbale ya cikho ca ukali wanga; iwe sudzamwa ico kawirinso.

23 Ndidzaciika m'dzanja la iwo amene abvutitsa iwe; amene anena ku moyo wako, Gwada pansi kuti ife tipite; ndipo iwe wagonetsa pamsana pako monga pansi, ndi monga khwalala kwa iwo amene apita pamenepo.

52

1 Galamuka galamuka, tabvala mphamvu zako, Ziyoni; tabvala zobvala zako zokongola, Yerusalemu, mzinda wopatulika; pakuti kuyambira tsopano sadzalowanso kwa iwe wosadulidwa ndi wodetsedwa.

2 Dzisanse pfumbi; uka, khala tsonga, Yerusalemu; udzimasulire maunyolo a pakhosi pako, iwe mwana wamkazi wam'nsinga wa Ziyoni.

3 Pakuti atero Yehova, Inu munagulitsidwa cabe, ndipo mudzaomboledwa opanda ndalama.

4 Pakuti Ambuye Yehova atero, Anthu anga ananka ku Aigupto poyamba paja, kukakhala kumeneko; ndipo Asuri anawatsendereza popanda cifukwa.

5 Cifukwa cace kodi ndicitenji pano? ati Yehova; popeza anthu anga acotsedwa popanda kanthu? akuwalamulira awaliritsa, ati Yehova; ndipo dzina langa licitidwa mwano tsiku lonse kosalekeza.

6 Cifukwa cace anthu anga adzadziwa dzina langa; cifukwa cacersiku limenelo iwo adzadziwa kuti Ine ndine amene ndinena; taonani, ndine pano.

7 Ha, akongolatu pamapiri mapazi a iye amene adza ndi uthenga wabwino, amene abukitsa mtendere, amene adza ndi uthenga wabwino wa zinthu zabwino, amene abukitsa cipulumutso; amene ati kwa Ziyoni, Mulungu wako ndi mfumu.

8 Mau a alonda ako! akweza mau, ayimba pamodzi; pakuti adzaona maso ndi maso, pamene Yehova abwerera kudza ku Ziyoni.

9 Kondwani zolimba, yimbani pamodzi, inu malo abwinja a pa Yerusalemu; pakuti Yehova watonthoza mtima wa anthu ace, waombola Yerusalemu.

10 Yehova wabvula mkono wace woyera pamaso pa amitundu onse; ndi malekezero onse a dziko lapansi adzaona cipulumutso ca Mulungu wathu.

11 Cokani inu, cokani inu, turukani ku Babulo; musakhudze kanthu kodetsa; turukani pakati pace, khalani okonzeka, inu amene munyamula zotengera za Yehova.

12 Pakuti simudzacoka mofulumira, kapena kunka mothawa; pakuti Yehova adzakutsogolerani, ndi Mulungu wa Israyeli adzadikira pambuyo panu.

13 Taonani, Mtumiki wanga adzacita mwanzeru; adzakwezedwa ndi kutukulidwa pamwamba, nadzakhala pamwambamwamba.

14 Monga ambiri anazizwa ndi iwe Israyeli, momwemo nkhope yace yaipitsidwa ndithu, kupambana munthu ali yense, ndi maonekedwe ace kupambana ana a anthu;

15 momwemonso Iye adzawazawaza mitundu yambiri; mafumu adzamtsekera Iye pakamwa pao; pakuti cimene sicinauzidwa kwa iwo adzaciona, ndi cimene iwo sanamva adzazindikira.

53

1 Ndani wamvera uthenga wathu? Ndi mkono wa Yehova wabvumbulukira yani?

2 Pakuti ameneyo adzaphuka pamaso pace ngati mtengo wanthete, ndi ngati muzu womera m'nthaka youma; Iye alibe maonekedwe, pena kukongola; ndipo pamene timuona palibe kukongola kuti timkhumbe.

3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wazisoni, ndi wodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu wombisira anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamlemekeza.

4 Zoonadi Iye ananyamula zowawa zathu, ndi kusenza zisoni zathu; koma ife tinamuvesa wokhomedwa wokanthidwa ndi Mulungu, ndi wobvutidwa.

5 Koma Iye analasidwa cifukwa ca zolakwa zathu, natundudzidwa cifukwa ca mphulupulu zathu; cilango cotitengera ife mtendere cinamgwera Iye; ndipo ndi mikwingwirima yace ife taciritsidwa.

6 Tonse tasocera ngati nkhosa; tonse tayenda yense m'njira ya mwini yekha; ndipo Yehova anaika pa Iye mphulupulu ya ife tonse.

7 Iye anatsenderezedwa koma anadzicepetsa yekha osatsegula pakamwa pace; ngati nkhosa yotsogoleredwa kukaphedwa, ndi ngati mwana wa nkhosa amene ali du pamaso pa omsenga, motero sanatsegula pakamwa pace.

8 Anacotsedwa ku cipsinjo ndi ciweruziro; ndipo ndani adzafotokoza nthawi ya moyo wace? pakuti walikhidwa kunja kuno; cifukwa ca kulakwa kwa anthu anga Iye anakhomedwa.

9 Ndipo anaika manda ace pamodzi ndi oipa, ndi pamodzi ndi olemera mu imfa yace, ngakhale Iye sanacita ciwawa, ndipo m'kamwa mwace munalibe cinyengo.

10 Koma kunakomera Yehova kumtundudza; anammvetsa zowawa; moyo wace ukapereka nsembe yoparamula, Iye adzaona mbeu yace, adzatanimphitsa masiku ace; ndipo comkondweretsa Yehova cidzakula m'manja mwace.

11 Iye adzaona zotsatira mabvuto a moyo wace, nadzakhuta nazo; ndi nzeru zace mtumiki wanga wolungama adzalungamitsa ambiri, nadzanyamula mphulupulu zao.

12 Cifukwa cace ndidzamgawira gawo ndi akuru; ndipo adzagawana ndi amphamvu zofunkha; pakuti Iye anathira moyo wace kuimfa; ndipo anawerengedwa pamodzi ndi olakwa; koma ananyamula macimo a ambiri, napembedzera olakwa.

54

1 Yimba, iwe wouma, amene sunabala; yimba zolimba ndi kupfuula zolimba, iwe amene sunabala mwana; pakuti ana a mfedwa acuruka koposa ana a mkazi wokwatibwa ndi mwamuna, ati Yehova.

2 Kuza malo a hema wako, afunyulule zinsaru za mokhalamo iwe; usaleke, tanimphitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.

3 Pakuti iwe udzafalikira ponse pa dzanja lamanja ndi lamanzere, ndipo mbeu yako idzalandira amitundu colowa cao, ndi kukhalitsa anthu m'mabwinja.

4 Usaope, pakuti sudzakhala ndi manyazi; usasokonezedwe, pakuti sudzacitidwa manyazi; pakuti udzaiwala manyazi a ubwana wako, ndi citonzo ca umasiye wako sudzacikumbukiranso.

5 Pakuti Mlengi wako ndiye mwamuna wako; Yehova wa makamu ndiye dzina lace; ndi Woyera wa Israyeli ndiye Mombolo wako; Iye adzachedwa Mulungu wa dziko lonse lapansi.

6 Pakuti Yehova wakuitana iwe monga mkazi wakusiyidwa ndi wosauka m'mzimu, ngakhale mkazi wa ubwana wocotsedwa, ati Mulungu wako.

7 Kamphindi kakang'ono ndakusiya iwe, koma ndi cifundo cambiri ndidzakusonkhanitsa.

8 M'kukwiya kwa kusefukira ndinakubisira nkhope yanga kamphindi; koma ndi kukoma mtima kwa cikhalire ndidzakucitira cifundo, ati Yehova Mombolo wako.

9 Pakuti kumeneku kuli kwa Ine monga madzi a Nowa; pakuti monga ndinalumbira kuti madzi a Nowa sadzamizanso pa dziko lapansi, momwemo ndinalumbira kuti sindidzakukwiyira iwe, pena kukudzudzula.

10 Pakuti mapiri adzacoka, ndi zitunda zidzasunthika; koma kukoma mtima kwanga sikudzakucokera iwe, kapena kusunthika cipangano canga ca mtendere, ati Yehova amene wakucitira iwe cifundo.

11 Iwe wosautsidwa, wobelukabeluka ndi namondwe, wosatonthola mtima, taona, ndidzakhazika miyala yako m'maanga-maanga abwino, ndi kukhazika maziko ako ndi masafiro.

12 Ndipo ndidzamanga mazenera ako ndi miyala yofiira, ndi zipata zako ndi bareketi, ndi malire ako onse ndi miyala yokondweretsa.

13 Ndipo ana ako onse adzaphunzitsidwa ndi Yehova; ndipo mtendere wa ana ako udzakhala waukulu.

14 M'cilungamo iwe udzakhazikitsidwa, udzakhala kutari ndi cipsinjo, pakuti sudzaopa; udzakhala kutari ndi mantha, pakuti sadzafika cifupi ndi iwe.

15 Taona, iwo angasonkhanitse pamodzi, koma si ndi Ine; amene ali yense adzasonkhana pamodzi akangane ndi iwe adzagwa cifukwa ca iwe.

16 Taona, ndalenga wacipala amene abvukuta moto wamakala, ndi kuturutsamo cida ca nchito yace; ndipo ndalenga woononga kuti apasule.

17 Palibe cida cosulidwira iwe cidzapindula; ndipo lilime lonse limene lidzakangana nawe m'ciweruzo udzalitsutsa. Ici ndi colowa ca atumiki a Yehova, ndi cilungamo cao cimene cifuma kwa Ine, ati Yehova.

55

1 Inu nonse, inu akumva ludzu, idzani kumadzi; ndi osowa ndarama idzani inu mugule mudye; inde idzani, mugule vinyo ndi mkaka opanda ndarama ndi opanda mtengo wace.

2 Bwanji inu mulikutayira ndarama cinthu cosadya, ndi kutayira malipiro anu zosakhutitsa? Mverani Ine mosamalitsa, nimudye cimene ciri cabwino, moyo wanu nubondwere ndi zonona.

3 Cherani Lhutu lanu, mudze kwa Ine, imvani, mzimu wanu nudzakhala ndi moyo; ndipo ndidzapangana nanu cipangano cosatha, ndico zifundo zoona za Davide.

4 Taonani, ndampereka iye akhale mboni ya anthu, wotsogolera ndi wolamulira anthu.

5 Taona, iwe udzaitana mtundu umene sunaudziwa, ndi mtundu umene sunakudziwa udzakuthamangira, cifukwa ca Yehova Mulungu wako, ndi cifukwa ca Woyera wa Israyeli; pakuti Iye wakukometsa.

6 Funani Yehova popezeka Iye, itanani Iye pamene ali pafupi;

7 woipa asiye njira yace, ndi munthu wosalungama asiye maganizo ace, nabwere kwa Yehova; ndipo Yehova adzamcitira cifundo; ndi kwa Mulungu wathu, pakuti Iye adzakhululukira koposa.

8 Pakuti maganizo anga sali maganizo anu, ngakhale njira zanu siziri njira zanga, ati Yehova.

9 Pakuti monga kumwamba kuli kutari ndi dziko lapansi, momwemo njira zanga ziri zazitari kupambana njira zanu, ndi maganizo anga kupambana maganizo anu.

10 Pakuti monga mvula imagwa pansi ndi matalala, kucokera kumwamba yosabwerera komweko, koma ikhamiza nthaka ndi kuibalitsa, ndi kuiphukitsa, ndi kuipatsitsa mbeu kwa wobzyala, ndi cakudya kwa wakudya;

11 momwemo adzakhala mau anga amene aturuka m'kamwa mwanga, sadzabwerera kwa Ine cabe, koma adzacita cimene ndifuna, ndipo adzakula m'mene ndinawatumizira.

12 Pakuti inu mudzaturuka ndi kukondwa, ndi kutsogozedwa ndi mtendere; mapiri ndi zitunda, zidzayimba zolimba pamaso panu, ndi mitengo yonse ya m'thengo idzaomba m'manja mwao.

13 M'malo mwa mithethe mudzaturuka mtengo wamlombwa; ndi m'malo mwa lunguzi mudzamera mtengo wamcisu; ndipo cidzakhala kwa Yehova ngati mbiri, ngati cizindikiro cosatha, cimene sicidzalikhidwa.

56

1 Atero Yehova, Sungani inu ciweruziro, ndi kucita cilungamo; pakuti cipulumutso canga ciri pafupi kudza, ndi cilungamo canga ciri pafupi kuti cib zumbulutsidwe,

2 Wodala munthu amene acita ici, ndi mwana wa munthu amene agwira zolimba ici, amene asunga sabata osaliipitsa, nasunga dzanja lace osacita nalo coipa ciri conse.

3 Mlendo amene wadziphatika yekha kwa Yehova asanene, kuti, Yehova adzandilekanitsa ndithu ndi anthu ace; pena mfule asanene, Taonani ine ndiri mtengo wouma.

4 Pakuti atero Yehova kwa mifule imene isunga masabata, nisankha zinthu zimene zindikondweretsa Ine, nigwira zolimba cipangano canga,

5 Kwa iyo ndidzapatsa m'nyumba yanga ndi m'kati mwa makoma anga malo, ndi dzina loposa la ana amuna ndi akazi; ndidzawapatsa dzina lacikhalire limene silidzadulidwa.

6 Alendonso amene adziphatika okha kwa Yehova, kuti amtumikire Iye, ndi kukonda dzina la Yehova, akhale atumiki ace, yense amene asunga sabata osaliipitsa, nagwira zolimba cipangano canga;

7 naonso ndidzanka nao ku phiri langa lopatulika, ndi kuwasangalatsa m'nyumba yanga yopemphereramo; zopereka zao zopsereza ndi nsembe zao zidzalandiridwa pa guwa la nsembe langa; pakuti nyumba yanga idzachedwa nyumba yopemphereramo anthu onse.

8 Ambuye Yehova amene asonkhanitsa otayika a Israyeli ati, Komabe ndidzasonkhanitsa ena kwa iye, pamodzi ndi osonkhanitsidwa ace ace.

9 Inu zirombo zonse za m'thengo, idzani kulusa, inde zirombo inu nonse za m'nkhalango.

10 Alonda ace ali akhungu, iwo onse ali opanda nzeru; iwo onse ali agaru acete, osatha kuuwa; kungolota, kugona pansi, kukonda kugona tulo.

11 Inde agaru ali osusuka, sakhuta konse; amenewa ali abusa osazindikira; iwo onse atembenukira ku njira zao, yense kutsata phindu lace m'dera lace.

12 Idzani inu, ati iwo, ndidzatengera vinyo, ndipo tidzakhuta cakumwa caukali; ndipo mawa kudzakhala monga tsiku lalero, tsiku lalikuru loposa ndithu.

57

1 Wolungama atayika, ndipo palibe munthu wosamalirapo; ndipo anthu acifundo atengedwa, palibe wolingalira kuti wolungama acotsedwa pa coipa cirinkudza.

2 Iye alowa mumtendere, iwo apuma pa mphasa zao, yense woyenda moongoka.

3 Koma sendererani kuno cifupi, inu ana amuna a watsenga, mbeu yacigololo ndi yadama.

4 Ndiye yani mudzikondweretsa momseka? Ndani mulikumyasamira kukamwa, ndi kumturutsira lilime? Kodi inu simuli ana akulakwa, mbeu yonama?

5 Inu amene muutsa zilakolako zanu pakati pa mathundu, patsinde pa mitengo yonse ya gudugudu, amene mupha ana m'zigwa pansi pa mapanga a matanthwe?

6 Pakuti pa miyala yosalala ya m'cigwa pali gawo lako; iyo ndiyo gawo lako; ndiyo imene unaitsanulirira nsembe yothira, ndi kupereka nsembe yaufa. Kodi ndidzapembedzedwa pa zinthu zimenezi?

7 Pamwamba pa phiri lalitaritari unayala mphasa yako; kumenekonso wakwera kukapereka nsembe.

8 Ndi kumbuyo kwa zitseko ndi mphuthu waimiritsa cikumbutso cako, pakuti wadzionetsa wekha kwa wina, wosati kwa Ine; ndipo wakwerako, wakuza mphasa yako, ndi kupangana nao pangano; unakonda mphasa yao kumene unaiona.

9 Ndipo unanka kwa mfumu, utadzola mafuta ndi kucurukitsa zonunkhira zako; ndipo unatumiza atumwi ako kutari; ndipo wadzicepetsa wekha kufikira kunsi ku manda.

10 Unatopa ndi njira yako yaitari; koma sunanene, Palibe ciyembekezo; iwe wapeza moyo wa dzanja lako; cifukwa cace sunalefuka.

11 Ndipo ndi yani amene wamuopa ndi kucita naye mantha, kuti wanama, osandikumbukira Ine, kapena kundisamalira? Kodi Ine sindinakhala cete nthawi yambiri, ndipo iwe sunandiopa Ine konse?

12 Ndidzaonetsa cilungamo cako ndi nchito zako sudzapindula nazo.

13 Pamene pakupfuula iwe akupulumutse amene unawasonkhanitsa; koma mphepo idzawatenga, mpweya udzacotsa onse; koma iye amene andikhulupirira Ine adzakhala ndi dziko, nadzakhala naco colowa m'phiri langa lopatulika.

14 Ndipo adzanena, Undani, undani, konzani njira, cotsani cokhumudwitsa m'njira mwa anthu anga.

15 Pakuti atero Iye amene ali wamtari wotukulidwa, amene akhala mwacikhalire, amene dzina lace ndiye Woyera, Ndikhala m'malo atari ndi oyera, pamodzi ndi yense amene ali wa mzimu wosweka ndi wodzicepetsa, kutsitsimutsa mzimu wa odzicepetsa, ndi kutsitsimutsa mtima wa osweka.

16 Pakuti sindidzatsutsana ku nthawi zonse, sindidzakwiya masiku onse; pakuti mzimu udzalefuka pamaso pa Ine, ndi miyoyo imene ndinailenga.

17 Cifukwa ca kuipa kwa kusirira kwace ndinakwiya ndi kummenya iye; ndinabisa nkhope yanga, ndipo ndinakwiya; ndipo iye anankabe mokhota m'njira ya mtima wace.

18 Ndaona njira zace, ndipo ndidzamciritsa; ndidzamtsogoleranso, ndi kumbwezera iye ndi olira maliro ace zotonthoza mtima.

19 Ndilenga cipatso ca milomo, Mtendere, mtendere kwa iye amene ali kutari, ndi kwa iye amene ali cifupi, ati Yehova; ndipo ndidzamciritsa iye.

20 Koma oipa ali ofanana ndi nyanja yowinduka; pakuti siingapume, ndi madzi ace autsa matope ndi ubve.

21 Palibe mtendere, ati Mulungu wanga, kwa oipa.

58

1 Pfuula zolimba, usalekerere, kweza mau ako ngati lipenga, ndi kuwafotokozera anthu anga colakwa cao, ndi banja la Yakobo macimo ao.

2 Koma iwo andifuna Ine tsiku ndi tsiku, ndi kukondwera kudziwa njira zanga; monga mtundu wa anthu ocita cilungamo, osasiya cilangizo ca Mulungu wao, iwo andipempha Ine zilangizo zolungama, nakondwerera kuyandikira kwa Mulungu.

3 Amati, Bwanji ife tasala kudya, ndipo Inu simuona? ndi bwanji ife tabvutitsa moyo wathu, ndipo Inu simusamalira? Taonani, tsiku la kusala kudya kwanu inu mupeza kukondwerera kwanu, ndi kutsendereza anchito anu onse.

4 Taonani, inu musala kudya kuti mukangane ndi kutsutsana ndi kukantha ndi nkhonya yoipa; inu simusala kudya tsiku lalero kuti mumveketse mau anu kumwamba.

5 Kodi kusala kudya koteroko ndiko ndinakusankha? tsiku lakubvutitsa munthu moyo wace? Kodi ndiko kuweramitsa mutu wace monga bango, ndi kuyala ciguduli ndi phulusa pansi pace? Kodi uyesa kumeneko kusala kudya, ndi tsiku lobvomerezeka kwa Yehova?

6 Kodi kumeneku si kusala kudya kumene ndinakusankha: kumasula nsinga za zoipa, ndi kumasula zomanga gori, ndi kuleka otsenderezedwa amuke mfulu, ndi kuti mutyole magori onse?

7 Kodi si ndiko kupatsa cakudya cako kwa anjala, ndi kuti ubwere nao kunyumba kwako aumphawi otayika? pakuona wamalisece kuti umbveke, ndi kuti usadzibisire wekha a cibale cako?

8 Pomwepo kuunika kwako kudzawalitsa monga m'mawa, ndi kucira kwako kudzaonekera msanga msanga; ndipo cilungamo cako cidzakutsogolera; ulemerero wa Yehova udzakhala wocinjiriza pambuyo pako.

9 Pamenepo udzaitana, ndipo Yehova adzayankha; udzapfuula ndipo Iye adzati, Ndine pano. Ngati ucotsa pakati pa iwe gori, kukodolana moipa, ndi kulankhula moipa,

10 ndipo ngati upereka kwa wanjala cimene moyo Iwako umakhumba, ndi kukhutitsa moyo wobvutidwa, pomwepo kuunika kwako kudzauka mumdima, ndipo usiku wako udzanga usana;

11 ndipo Yehova adzakutsogolera posalekai, ndi kukhutitsa moyo wako m'cirala, ndi kulimbitsa mafupa ako; ndipo udzafanana ndi munda wothirira madzi, ndi kasupe wamadzi amene madzi ace saphwa konse.

12 Ndipo iwo amene adzakhala a iwe adzamanga malo akale abwinja; udzautsa maziko a mibadwo yambiri; udzachedwa Wokonza pogumuka, Wakubwezera njira zakukhalamo.

13 Ukaletsa phazi lako pa Sabata, ndi kusiya kucita kukondwerera kwako tsiku: langa lopatulika, ndi kuyesa Sabata tsiku lokondwa lopatulika la Yehova, lolemekezeka, ndipo ukalilemekeza ilo, osacita njira zako zokha, osafuna kukondwa kwako kokha, osalankhula mau ako okha;

14 pomwepo udzakondwa mwa Yehova; ndipo Ine ndidzakuyendetsa pa misanje ya dziko lapansi; ndipo ndidzakudyetsa colowa ca kholo lako Yakobo; pakuti pakamwa pa Yehova pananenapo.

59

1 Taonani, mkono wa Yehova sufupika, kuti sungathe kupulumutsa; khutu lace siliri logontha, kuti silingamve;

2 koma zoipa zanu zakulekanitsani inu ndi Mulungu wanu; ndipo macimo anu abisa nkhope yace kwa inu, kuti Iye sakumva.

3 Pakuti manja anu adetsedwa ndi mwazi, ndi zala zanu ndi mphulupulu, milomo yanu yanena zonama, lilime lanu lilankhula moipa.

4 Palibe woturutsa mlandu molungama, ndipo palibe wonena zoona; iwo akhulupirira mwacabe, nanena zonama; iwo atenga kusayeruzika ndi kubala mphulupulu,

5 Iwo afungatira mazira a mamba aswetse, naluka ukonde wa tandaude; iye amene adya mazira ace amafa, ndi coswanyikaco cisweka nicikhala songo.

6 Maukonde ao sadzakhala zobvala, sadzapfunda nchito zao; nchito zao ziri nchito zoipa, ndi ciwawa ciri m'manja mwao.

7 Mapazi ao athamangira koipa, ndipo iwo afulumira kukhetsa mwazi wosacimwa; maganizo ao ali maganizo oipa; bwinja ndi cipasuko ziri m'njira mwao.

8 Njira ya mtendere saidziwa, ndipo palibe ciweruziro m'mayendedwe mwao; akhotetsa njira zao; ali yense ayenda m'menemo sadziwa mtendere.

9 Cifukwa cace ciweruziro ciri patari ndi ife, ndi cilungamo sicitipeza; tiyang'anira kuunika, koma taona mdima; tiyang'anira kuyera, koma tiyenda m'usiku.

10 Tiyambasira khoma ngati wakhungu, inde tiyambasa monga iwo opanda maso; tipunthwa usana monga m'cizirezire; tiri m'malo amdima ngati akufa.

11 Tonse tibangula ngati zirombo, ndi kulira maliro zolimba ngati nkhunda; tiyang'anira ciweruziro koma palibe; tiyang'anira cipulumutso koma ciri patari ndi ife.

12 Pakuti zolakwa zathu zacuruka pamaso pa Inu, ndipo macimo athu atineneza ife; pakuti zolakwa zathu ziri ndi ife, ndipo zoipa zathu tizidziwa;

13 ndizo kulakwabe ndi kukanabe Yehova, ndi kuleka kutsata Mulungu wathu, kulankhula zotsendereza ndi kupanduka, kuganizira ndi kunena pakamwa mau akunyenga oturuka mumtima.

14 Ndipo ciweruziro cabwerera m'mbuyo, ndi cilungamo caima patari; pakuti coona cagwa m'khwalala, ndi kuongoka sikungalowe.

15 Inde coona cisoweka; iye amene asiya coipa, zifunkhidwa zace; ndipo Yehova anaona ici, ndipo cidamuipira kuti palibe ciweruzo.

16 Ndipo Iye anaona kuti palibe munthu, nazizwa kuti palibe wopembedzera; cifukwa cace mkono wace wace unadzitengera yekha cipulumutso; ndi cilungamo cace cinamcirikiza.

17 Ndipo anabvala cilungamo monga cida ca pacifuwa, ndi cisoti ca cipulumutso pamutu pace; nabvala zobvala zakubwezera cilango, nabvekedwa ndi cangu monga copfunda,

18 Monga mwa nchito zao momwemo Iye adzabwezera amaliwongo ace ukali, nadzabwezera adani ace cilango; nadzabwezeranso zisumbu cilango.

19 Comweco iwo adzaopa dzina la Yehova kucokera kumadzulo, ndi ulemerero wace kumene kuturukira dzuwa; pakuti pamene mdani adzafika ngati cigumula, mzimu wa Yehova udzamkwezera mbendera yomletsa.

20 Ndipo Mombolo adzafika ku Ziyoni, ndi kwa iwo amene atembenuka kusiya kulakwa mwa Yakobo, ati Yehova.

21 Ndipo kunena za. Ine, ili ndi pangano langa ndi iwo, ati Yehova; mzimu wanga umene uli pa iwe, ndi mau anga amene ndaika m'kamwa mwako sadzacoka m'kamwa mwako, pena m'kamwa mwa ana ako, pena m'kamwa mwa mbeu ya mbeu yako, ati Yehova, kuyambira tsopano ndi ku nthawi zonse.

60

1 Nyamuka, wala, pakuti kuunika kwake kwafika, ndi ulemerero wa Yehova wakuturukira.

2 Pakuti taona, mdima udzaphimba dziko lapansi, ndi mdima wa bii mitundu ya anthu; koma Yehova adzakuturukira, ndi ulemerero wace udzaoneka pa iwe.

3 Ndipo amitundu adzafika kwa kuunika kwako, ndi mafumu kwa kuyera kwa kuturuka kwake,

4 Tukula maso ako uunguze-unguze ndi kuona; iwo onse asonkhana pamodzi, adza kwa iwe; ana ako amuna adzacokera kutari, ndi ana ako akazi adzaleredwa pambali.

5 Pamenepo udzaona ndi kuunikidwa, ndipo mtima wako udzanthunthumira ndi kukuzidwa; pakuti unyinji wa nyanja udzakutembenukira, cuma ca amitundu cidzafika kwa iwe.

6 Gulu la ngamila lidzakukuta, ngamila zazing'ono za Midyani ndi Efa; iwo onsewo adzacokera ku Seba adzabwera nazo golidi ndi zonunkhira; ndipo adzalalikira matamando a Yehova.

7 Zoweta za Kedara zidzasonkhana kwa iwe, nkhosa zamphongo za Nebaioti zidzakutumikira; izo zidzafika ndi kulandiridwa pa guwa langa la nsembe; ndipo ndidzakometsa nyumba ya ulemerero wanga.

8 Ndani awa amene auluka ngati mtambo, ndi monga nkhunda ku mazenera ao?

9 Zoonadi, zisumbu zidzandilindira Ine; zidzayamba ndi ngalawa za Tarisi kutenga ana ako amuna kutari, golidi wao ndi siliva wao pamodzi nao, cifukwa ca dzina la Yehova Mulungu wako, ndi cifukwa ca Woyera wa Israyeli, popeza Iye wakukometsa iwe.

10 Ndipo alendo adzamanga malinga ako, ndi mafumu ao adzakutumikira; pakuti m'kukwiya kwanga ndinakantha, koma mokomera mtima ndidakucitira iwe cifundo.

11 Zipata zako zidzakhalabe zotseguka, sizidzatsekedwa usana pena usiku, kuti abwere naco kwa iwe cuma ca amitundu, ndi mafumu ao otsogozedwa nao pamodzi.

12 Pakuti mtundu ndi ufumu umene udzakana kukutumikira udzaonongeka; inde mitundu imeneyo idzasakazidwa ndithu.

13 Ulemerero wa Lebano udzafika kwa iwe; mtengo wamlombwa, mtengo wamkuyu ndi mtengo wanaphini pamodzi, kukometsera malo a kacisi wanga; ndipo ndidzacititsa malo a mapazi anga ulemerero.

14 Ndipo ana amuna a iwo amene anabvuta iwe adzafika, nadzakugwadira; ndipo iwo onse amene anakucepetsa iwe adzagwadira ku mapazi ako, nadzakucha iwe, Mudzi wa Yehova, Ziyoni wa Woyera wa Israyeli.

15 Ungakhale unasiyidwa ndi kudedwa, osapita munthu mwa iwe, Ine ndidzakusandutsa cangwiro cosatha, cokondweretsa ca mibadwo yambiri.

16 Iwe udzayamwanso mkaka wa amitundu, nudzayamwa bere la mafumu, nudzadziwa kuti Ine Yehova ndine mpulumutsi wako, ndi Mombolo wako, Wamphamvu wa Yakobo.

17 M'malo mwa mkuwa ndidzatenga golidi, ndi m'malo mwa citsulo ndidzatenga siliva, ndi m'malo mwa mtengo ndidzatenga mkuwa, ndi m'malo mwa miyala ndidzatenga citsulo; ndidzakuikira akapitao a mtendere, ndi oyang'anira nchito a cilungamo.

18 Ciwawa sicidzamvekanso m'dziko mwako, kupululutsa pena kupasula m'malire ako; koma udzacha malinga ako Cipulumutso, ndi zipata zako Matamando.

19 Dzuwa silidzakhalanso kuunika kwako usana, ngakhale mwezi sudzakuunikiranso kuti kuyere; koma Yehova adzakhala kwa iwe kuunika kosatha, ndi Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.

20 Dzuwa lako silidzalowanso, mwezi wako sudzanka kumidima; pakuti Yehova adzakhala kuunika kwako kosatha, ndi masiku a kulira maliro ako adzatha.

21 Anthu ako adzakhalanso onse olungama; dzikolo lidzakhala colowa cao ku nthawi zonse, nthambi yooka Ine, nchito ya manja anga, kuti Ine ndikuzidwe.

22 Wamng'ono adzasanduka cikwi, ndi wocepa adzasanduka mtundu wamphamvu; Ine Yehova ndidzafulumiza ici m'nthawi yace.

61

1 Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine; pakuti Yehova wandidzoza ine ndilalikire mau abwino kwa ofatsa; Iye wanditumiza ndikamange osweka mtima, ndikalalikire kwa am'nsinga mamasulidwe, ndi kwa omangidwakutsegulidwa kwa m'ndende;

2 ndikalalikire caka cokomera Yehova, ndi tsiku lakubwezera la Mulungu wathu; ndikatonthoze mtima wa onse amene akulira maliro;

3 ndikakonzere iwo amene alira maliro m'Ziyoni, ndi kuwapatsa cobvala kokometsa m'malo mwa phulusa, mafuta akukondwa m'malo mwa maliro, cobvala ca matamando m'malo mwa mzimu wopsinjika; kuti iwo achedwe mitengo ya cilungamo yakuioka Yehova, kuti Iye alemekezedwe.

4 Ndipo iwo adzamanga mabwinja akale, nadzamanga pa miunda yakale, nadzakonzanso midzi yopasuka, mabwinja a mibadwo yambiri.

5 Ndipo alendo adzaimirira ndi kudyetsa magulu ako, ndi anthu akunja adzakhala olima ako, ndi kukukonzera minda yamphesa.

6 Koma inu mudzachedwa ansembe a Yehova; anthu adzakuyesani inu atumiki a Mulungu wathu; inu mudzadya cuma ca amitundu, nimudzalowa mu ulemerero wao.

7 M'malo mwa manyazi anu, owirikiza; ndi citonzo iwo adzakondwera ndi gawo lao; cifukwa cace iwo adzakhala naco m'dziko mwao colowa cowirikiza, adzakhala naco cikondwerero cosatha.

8 Pakuti Ine Yehova ndikonda ciweruziro, ndida cifwamba ndi coipa; ndipo ndidzawapatsa mphotho yao m'zoonadi; ndipo ndidzapangana nao pangano losatha.

9 Ndipo ana ao adzadziwidwa mwa amitundu, ndi obadwa ao mwa anthu; onse amene awaona adzawazindikira kuti iwo ndiwo ana amene Yehova wadalitsa.

10 Ndidzakondwa kwambiri mwa Yehova, moyo wanga udzakondwerera mwa Mulungu wanga; pakuti Iye wandibveka ine ndi zobvala za cipulumutso, nandipfunda copfunda ca cilungamo, monga mkwati abvala nduwira, ndi monga mkwatibwi adzikometsa yekha ndi miyala yamtengo.

11 Pakuti monga dziko liphukitsa mphundu zace, ndi monga munda umeretsa zobzalamo, momwemo Ambuye Yehova adzaphukitsa cilungamo ndi matamando pamaso pa amitundu onse.

62

1 Cifukwa ca Ziyoni sindidzakhala cete, ndi cifukwa ca Yerusalemu sindidzapuma, kufikira cilungamo cace cidzaturuka monga kuyera, ndi cipulumutso cace monga nyali yoyaka.

2 Ndipo amitundu adzaona cilungamo cako, ndi mafumu onse ulemerero wako; ndipo udzachedwa dzina latsopano, limene m'kamwa mwa Yehova mudzachula.

3 Iwe udzakhalanso korona wokongola m'dzanja la Yehova, korona wacifumu m'dzanja la Mulungu wako.

4 Iwe sudzachedwanso Wosiyidwa; dziko lako silidzachedwanso Bwinja; koma iwe udzachedwa Hefiziba ndi dziko lako Beula; pakuti Yehova akondwera mwa iwe, ndipo dziko lako lidzakwatiwa.

5 Pakuti monga mnyamata akwatira namwali, momwemo ana ako amuna adzakukwama iwe; ndi monga mkwati akondwera ndi mkwatibwi, momwemo Mulungu wako adzakondwera nawe.

6 Ndaika alonda pa malinga ako, Yerusalemu; iwo sadzakhala cete usana pena usiku; inu akukumbutsa Yehova musakhale cete,

7 ndipo musamlole akhale cete, kufikira Iye atakhazikitsa naika Yerusalemu akhale tamando m'dziko lapansi.

8 Yehova analumbira pa dzanja lace lamanja, ndi mkono wace wamphamvu, Zoonadi, sindidzaperekanso tirigu wako akhale cakudya ca adani ako, ndipo alendo sadzamwa vinyo wako amene iwe unagwirira nchito;

9 koma iwo amene adzakolola adzadya ndi kutamanda Yehova; ndi iwo amene adzamchera adzamumwa m'mabwalo a kacisi wanga.

10 Pitani, pitani pazipata; konzani njira ya anthu; undani, undani khwalala; cotsani miyala, kwezani mbendera ya anthu.

11 Taonani, Yehova walalikira kufikira malekezero a dziko lapansi. Nenani kwa mwana wamkazi wa Ziyoni, Taona cipulumutso cako cifika; taona mphotho yace ali nayo, ndi nchito yace iri pamaso pace.

12 Ndipo iwo adzawacha Anthu opatulika, Oomboledwa a Yehova; ndipo iwe udzachedwa Wofunidwa, Mudzi wosasiyidwa.

63

1 Ndani uyu alinkudza kucokera ku Edomu, ndi zobvala zonika zocokera ku Bozira? uyu wolemekezeka m'cobvala cace, nayenda mu ukuru wa mphamvu zace? Ndine amene ndilankhula m'colungama, wa mphamvu yakupulumutsa,

2 Cophimba cako cifiiriranji, ndi zobvala zako zifanana bwanji ndi woponda mopondera mphesa?

3 Ndaponda ndekha mopondera mphesa, ndipo panalibe nane mmodzi wa mitundu ya anthu; inde ndinawaponda m'kukwiya kwanga, ndi kuwapondereza mu ukali wanga: ndi mwazi wa moyo wao unawazidwa pa zobvala zanga; ndipo ndadetsa copfunda canga conse.

4 Pakuti tsiku lakubwezera liri mumtima mwanga, ndi caka ca kuombola anthu anga cafika.

5 Ndipo ndinayang'ana, koma panalibe wothangata; ndipo ndinadabwa kuti panalibe wocirikiza; cifukwa cace mkono wanga wanga unanditengera cipulumutso, ndi ukali wanga unandicirikiza Ine.

6 Ndipo ndinapondereza anthu m'kukwiya kwanga, ndi kuwatswanya mu ukali wanga, ndi kutsanulira mwazi wa moyo wao.

7 Ndidzachula za cifundo cace ca Yehova, ndi matamando a Yehova, monga mwa zonse zimene Yehova wapereka kwa ife; ndi ubwino wace waukuru kwa banja la Israyeli, umene Iye wapereka kwa iwo, monga mwa cifundo cace, ndi monga mwa nchito zocuruka za cikondi cace.

8 Pakuti anati, Zoonadi iwo ndiwo anthu anga, ana amene sangacite monyenga; comweco Iye anali Mpulumutsi wao.

9 M'mazunzo ao onse Iye anazunzidwa, ndipo mthenga wakuimirira pamaso pace anawapulumutsa; m'kukonda kwace ndi m'cisoni cace Iye anawaombola, nawabereka nawanyamula masiku onse akale.

10 Koma iwo anapandukira ndi kumvetsa cisoni mzimu wace woyera, cifukwa cace Iye anasandulika mdani wao, nawathira nkhondo Iye yekha.

11 Pamenepo iwo anakumbukira masiku akale, Mose ndi anthu ace, nati, Ali kuti Iye amene anawaturutsa m'nyanja pamodzi ndi abusa a gulu lace? Ali kuti Iye amene anaika mzimu wace woyera pakati pao,

12 amene anayendetsa mkono wace waulemerero pa dzanja lamanja la Mose? amene anagawanitsa madzi pamaso pao, kuti adzitengere mbiri yosatha?

13 amene anawatsogolera kupitira mwa kuya monga kavalo m'cipululu osapunthwa iwo?

14 Monga ng'ombe zotsikira kucigwa mzimu wa Yehova unawapumitsa; comweco inu munatsogolera anthu anu kudzitengera mbiri yaulemerero.

15 Tayang'anani kunsi, taonani pokhala panu poyera, ndi pa ulemerero wanu, cangu canu ndi nchito zanu zamphamvu ziri kuti? mwanditsekerezera zofunafuna za mtima wanu ndi cisoni canu.

16 Pakuti Inu ndinu Atate wathu, ngakhale Abrahamu satidziwa ife, ndi Israyeli satizindikira ife. Inu Yehova ndinu Atate wathu, Mombolo wathu wacikhalire ndi dzina lanu.

17 Yehova bwanji mwatisoceretsa kusiya njira zanu, ndi kuumitsa mitima yathu tisakuopeni? Bwerani, cifukwa ca atumiki anu, mafuko a colowa canu.

18 Anthu anu opatulika anakhala naco kanthawi kokha; adani athu apondereza kacisi wanu wopatulika.

19 Ife takhala ngati iwo amene simunawalamulira konse, ngati iwo amene sanachedwa dzina lanu.

64

1 Mwenzi mutang'amba kumwamba ndi kutsikira pansi, kuti mapiri agwedezeke pamaso panu;

2 monga pamene moto uyatsa zitsamba, ndi moto uwiritsa madzi; kudziwitsa kwa amaliwongo anu dzina lanu, kuti amitundu anthunthumire pamaso panu,

3 Pamene Inu munacita zinthu zoopsya, zimene ife sitinayang'anira, Inu munatsika, mapiri anagwedezeka pamaso panu.

4 Pakuti kuyambira kale anthu sanamve pena kumvetsa ndi khutu, ngakhale diso silinaone Mulungu wina popanda Inu, amene amgwirira nchito iye amene amlindirira Iye.

5 Inu mukomana ndi iye amene akondwerera, nacita cilungamo, iwo amene akumbukira Inu m'njira zanu; taonani Inu munakwiya, ndipo ife tinacimwa; takhala momwemo nthawi yambiri, kodi tidzapulumutsidwa?

6 Pakuti ife tonse takhala ngati wina amene ali wosakonzeka; ndi zolungama zathu zonse ziri ngati cobvala codetsedwa; ndipo ife tonse tifota monga tsamba, ndi zoipa zathu zitiuluza monga mphepo.

7 Ndipo palibe amene aitana dzina lanu, amene adzikangamiza yekha kugwiritsa Inu; pakuti Inu mwatibisira nkhope yanu, ndipo mwatinyeketsa ndi zoipa zathu.

8 Koma tsopano, Yehova, Inu ndinu Atate wathu; ife tiri dongo, ndipo Inu ndinu Muumbi wathu; ndipo ife tonse tiri nchito ya dzanja lanu.

9 Musakwiye kopambana, Yehova, musakumbukire zoipa nthawi zonse; taonani, yang'anani ife, tikupembedzani Inu, ife tonse tiri anthu anu.

10 Midzi yanu yopatulika yasanduka cipululu, Ziyoni wasanduka cipululu, Yerusalemu wasanduka bwinja.

11 Nyumba yathu yopatulika ndi yokongola, m'mene makolo athu anakutamandani Inu, yatenthedwa ndi moto; ndi zinthu zathu zonse zokondweretsa zapasuka.

12 Kodi mudzadziletsa pa zinthuzi, Yehova? Kodi Inu mudzakhala cete ndi kutibvutitsa ife zolimba?

65

1 Iwo amene sanafunsa za Ine andifunafuna; ndi iwo amene sanandipwaira andipeza; ndinati, Taonani Ine, taonani Ine, kwa mtundu umene sunachula dzina langa.

2 Ndatambasulira manja anga tsiku lonse kwa anthu opanduka, amene ayenda m'njira mosati mwabwino, kutsata maganizo ao ao;

3 anthu amene andiputa Ine kumaso kwanga nthawi zonse, apereka nsembe m'minda, nafukizira zonunkhira panjerwa;

4 amene akhala pakati pa manda, ndi kugona m'malo am'tseri; amene adya nyama ya nkhumba, ndi msuzi wa zinthu zonyansa uli m'mbale zao;

5 amene ati, Ima pa wekha, usadze cifupi ndi ine, pakuti ine ndiri woyera kupambana iwe; amenewa ndiwo utsi m'mphuno mwanga, moto woyaka tsiku lonse.

6 Taonani, calembedwa pamaso panga; sindidzakhala cete, koma ndidzabwezera, inde ndidzabwezera pa cifuwa cao,

7 zoipa zanu zanu pamodzi ndi zoipa za makolo anu, ati Yehova, amene anafukiza zonunkhira pamapiri, nandicitira mwano pazitunda; cifukwa cace Ine ndidzayesa nchito yao yakale ilowe pa cifuwa cao.

8 Atero Yehova, Monga vinyo watsopano apezedwa m'tsango, ndipo wina ati, Usaliononge, pakuti muli mdalitso m'menemo, momwemo ndidzacita cifukwa ca atumiki anga, kuti ndisawaononge onse.

9 Ndipo ndidzaturutsa mbeu mwa Yakobo, ndi mwa Yuda wolowa nyumba wa mapiri anga; ndipo osankhidwa anga adzalandira colowa cao, ndi atumiki anga adzakhala kumeneko.

10 Ndipo Saroni adzakhala podyetsera nkhosa, ndi cigwa ca Akori cidzakhala pogona zoweta kwa anthu anga amene andifuna Ine.

11 Koma inu amene mwasiya Yehova, amene mwaiwala phiri langa lopatulika, ndi kukonzera mlungu wamwai gome, ndi kudzazira mlungu waimfa zikho za vinyo wosanganiza;

12 ndidzasankhiratu inu kulupanga, ndipo inu nonse mudzagwada ndi kuphedwa; pakuti pamene ndinaitana, inu simunayankhe; pamene ndinanena, simunamve; koma munacita coipa m'maso mwanga, ndi kusankha cimene Ine sindinakondwera naco.

13 Cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Taonani atumiki anga adzadya, koma inu mudzakhala ndi njala; taonani, atumiki anga adzamwa, koma inu mudzakhala ndi ludzu; taonani, atumiki anga adzasangalala, koma inu mudzakhala ndi manyazi;

14 taonani, atumiki anga adzayimba ndi mtima wosangalala, koma inu mudzalira ndi mtima wacisoni; ndipo mudzapfuula cifukwa ca kusweka mzimu.

15 Ndipo mudzasiya dzina lanu likhale citemberero kwa osankhidwa anga, ndipo Ambuye Yehova adzakupha iwe, nadzacha atumiki ace dzina lina;

16 comweco iye amene adzidalitsa yekha m'dziko lapansi, adzadzidalitsa yekha mwa Mulungu woona; ndipo iye amene alumbira m'dziko lapansi adzalumbira pa Mulungu woona; popeza zobvuta zoyamba zaiwalika, ndi popeza zabisalika kumaso kwanga.

17 Pakuti taonani, ndilenga kumwamba kwa tsopano ndi dziko lapansi latsopano; ndipo zinthu zakale sizidzakumbukika, pena kulowa mumtima.

18 Koma khalani inu okondwa ndi kusangalala ku nthawi zonse ndi ici ndicilenga; pakuti taonani, ndilenga Yerusalemu wosangalala, ndi anthu ace okondwa.

19 Ndipo ndidzasangalala m'Yerusalemu, ndi kukondwera mwa anthu anga; ndipo mau akulira sadzamvekanso mwa iye, pena mau akupfuula.

20 Sipadzakhalanso khanda la masiku, pena munthu wokalamba osakwanitsa masiku ace; pakuti mwana adzafa wa zaka zana limodzi; ndipo wocimwa pokhala wa zaka zana limodzi adzatembereredwa.

21 Ndipo iwo adzamanga nyumba ndi kukhalamo; ndipo iwo adzanka minda yamphesa, ndi kudya zipatso zace.

22 Iwo sadzamanga, ndi wina kukhalamo; iwo sadzanka, ndi wina kudya; pakuti monga masiku a mtengo adzakhalamasiku a anthu anga; ndi osankhidwa anga adzasangalala nthawi zambiri ndi nchito za manja ao.

23 Iwo sadzagwira nchito mwacabe, pena kubalira tsoka; pakuti iwo ndiwo mbeu ya odalitsidwa a Yehova, ndi obadwa ao adzakhala pamodzi ndi iwo.

24 Ndipo padzakhala kuti iwo asanaitane Ine, ndidzayankha; ndipo ali cilankhulire, Ine ndidzamva.

25 Mmbulu ndi mwana wa nkhosa zidzadyera pamodzi; ndi mkango udzadya udzu ngati ng'ombe; ndi pfumbi lidzakhala cakudya ca njoka; sizidzapwetekana, kapena kusakazana m'phiri langa lonse lopatulika, ati Yehova.

66

1 Atero Yehova, Kumwamba ndi mpando wanga wacifumu, ndi dziko lapansi ndi coikapo mapazi anga; mudzandimangira Ine nyumba yotani? ndi malo ondiyenera kupumamo ali kuti?

2 Pakuti zonsezi mkono wanga wazilenga, momwemo zonsezi zinaoneka, ati Yehova; koma ndidzayang'anira munthu uyu amene ali waumphawi, ndi wa mzimu wosweka, nanthunthumira ndi mau anga.

3 Wakupha ng'ombe alingana ndi wakupha munthu; iye wapereka nsembe ya mwana wa nkhosa alingana ndi wotyola khosi la garu; wothira nsembe yaufa akunga wothira mwazi wa nkhumba; wofukiza conunkhira akunga wodalitsa fano; inde iwo asankha njira zao zao, ndipo moyo wao ukondwerera m'zonyansa zao;

4 Inenso ndidzasankha zodzinyenga nazo, ndipo ndidzatengera mantha ao pa iwo; pakuti pamene ndinaitana, panalibe woyankha; pamene ndinalankhula, iwo sanamva konse; koma anacita coipa m'maso mwanga, ndi kusankha cimene ndisanakondwere naco.

5 Imvani mau a Yehova, inu amene munthunthumira ndi mau ace; abale anu amene akudani inu, amene anaponya inu kunja cifukwa ca dzina langa, iwo anati, Yehova alemekezedwe, kuti ife tione kusangalala kwanu; koma iwo adzakhala ndi manyazi.

6 Mau a phokoso acokera m'mudzi, mau ocokera m'Kacisi, mau a Yehova amene abwezera adani ace cilango.

7 Mkazi asanamve zowawa, anabala mwana; kupweteka kwace kusanadze, anabala mwana wamwamuna.

8 Ndani anamva kanthu kotereko? ndani anaona zinthu zoterezo? Kodi dziko lidzabadwa tsiku limodzi? Kodi mtundu udzabadwa modzidzimutsa? pakuti pamene Ziyoni anamva zowawa, pomwepo anabala ana ace.

9 Kodi Ine ndidzafikitsira mkazi nthawi yakutula osamtulitsa? ati Yehova; kodi Ine amene ndibalitsa ndidzatseka mimba? ati Mulungu wako.

10 Sangalalani inu pamodzi ndi Yerusalemu, ndipo kondwani cifukwa ca iye, inu nonse amene mumkonda; sangalalani kokondwa pamodzi ndi iye, inu nonse akumlira maliro;

11 kuti mukayamwe ndi kukhuta ndi mabere a zitonthozo zace; kuti mukafinye mkaka ndi kukondwerera ndi unyinji wa ulemerero wace.

12 Pakuti atero Yehova, Taonani ndidzamfikitsira mtendere ngati mtsinje, ndi ulemerero wa amitundu ngati mtsinje wosefukira. Inu mudzayamwa, ndi kunyamulidwa pambali, ndi kululuzidwa pa maondo,

13 Monga munthu amene amace amtonthoza mtima, momwemo ndidzatonthoza mtima wanu; ndipo mudzatonthozedwa mtima m'Yerusalemu.

14 Ndipo mudzaciona, ndipo mtima wanu udzasangalala, ndipo mafupa anu adzakula ngati msipu; ndipo dzanja la Yehova lidzadziwika ndi atumiki ace, ndipo adzakwiyira adani ace.

15 Pakuti taonani, Yehova adzafika m'moto, ndi magareta ace adzafanana ndi kabvumvulu; kubwezera mkwiyo wace ndi ukali, ndi kudzudzula ndi malawi amoto,

16 Pakuti Yehova adzatsutsana ndi moto, ndi lupanga lace, ndi anthu onse; ndi ophedwa a Yehova adzakhala ambiri.

17 Iwo amene adzipatulitsa nadziyeretsa, kuti amuke kuminda tsatane tsatane, ndi kudya nyama ya nkhumba, ndi conyansa, ndi mbewa, adzathedwa pamodzi, ati Yehova.

18 Pakuti Ine ndidziwa nchito zao ndi maganizo ao; nthawi ikudza yakudzasonkhanitsa Ine a mitundu yonse ndi zinenedwe zonse, ndipo adzafika nadzaona ulemerero wanga.

19 Ndipo ndidzaika cizindikiro pakati pao, ndipo ndidzatumiza onse amene apulumuka mwa iwo kwa amitundu, kwa Tarisi, kwa Puli ndi kwa Aludi, okoka uta kwa Tubali ndi Yavana, ku zisumbu zakutari, amene sanamve mbiri yanga, ngakhale kuona ulemerero wanga; ndipo adzabukitsa ulemerero wanga pakati pa amitundu.

20 Ndipo iwo adzatenga abale anu onse mwa amitundu onse akhale nsembe ya kwa Yehova; adzabwera nao pa akavalo, ndi m'magareta, ndi m'macila, ndi pa nyuru, ndi pa ngamila, kudza ku phiri langa lopatulika ku Yerusalemu, ati Yehova, monga ana a Israyeli abwera nazo nsembe zao m'cotengera cokonzeka ku nyumba ya Yehova.

21 Ndipo ena a iwo ndidzawatenga akhale ansembe ndi Alevi, ati Yehova.

22 Pakuti monga m'mwamba mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano limene ndidzalenga, lidzakhalabe pamaso pa Ine, ati Yehova, momwemo adzakhalabe ana anu ndi dzina lanu.

23 Ndipo kudzakhala kuti kuyambira pa mwezi wokhala kufikira ku unzace, ndi kuyambira pa Sabata lina kufikira ku linzace, anthu onse adzafika kudzapembedzera pamaso pa Ine, ati Yehova.

24 Ndipo iwo adzaturuka ndi kuyang'ana mitembo ya anthu amene andilakwira Ine, pakuti mbozi yao sidzafa, pena moto wao sudzazimidwa; ndipo iwo adzanyansa anthu onse.