1

1 MIYAMBI ya Solomo mwana wa Davide, mfumu ya Israyeli.

2 Kudziwa nzeru ndi mwambo; Kuzindikira mau ozindikiritsa;

3 Kulandira mwambo wakusamalira macitidwe, Cilungamo, ciweruzo ndi zolunjika;

4 Kucenjeza acibwana, Kuphunzitsa mnyamata kudziwa ndi kulingalira;

5 Kuti wanzeru amve, naonjezere kuphunzira; Ndi kuti wozindikira afikire kuuphungu;

6 Kuzindikira mwambi ndi tanthauzo lace, Mau a anzeru, ndi zophiphiritsa zao.

7 Kuopa Yehova ndiko ciyambi ca kudziwa; Opusa anyoza nzeru ndi mwambo.

8 Mwananga, tamva mwambo wa atate wako, Ndi kusasiya cilangizo ca amako

9 Pakuti izi ndi korona wa cisomo pamtu pako, Ndi mkanda pakhosi pako.

10 Mwananga, akakukopa ocimwa usalole.

11 Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi, Tilalire osacimwa opanda cifukwa;

12 Tiwameze ali ndi moyo ngati manda, Ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;

13 Tidzapeza cuma conse ca mtengo wace, Tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;

14 Udzacita nafe maere, Tonse tidzakhala ndi cibeti cimodzi;

15 Mwananga, usayende nao m'njira; Letsa phazi lako ku mayendedwe ao;

16 Pakuti mapazi ao athamangira zoipa, Afulumira kukhetsa mwazi.

17 Pakuti kuchera msampha pamaso pa mbalame ndi cabe;

18 Ndipo awa abisalira mwazi wao wao, alalira miyoyo yao yao.

19 Mayendedwe a yense wopindula cuma monyenga ngotere; Cilanda moyo wa eni ace,

20 Nzeru ipfuula panja; Imveketsa mau ace pabwalo;

21 Iitana posonkhana anthu polowera pacipata; M'mudzi inena mau ace;

22 Kodi mudzakonda zacibwana kufikira liti, acibwana inu? Onyoza ndi kukonda kunyoza, Opusa ndi kuda nzeru?

23 Tembenukani pamene ndikudzudzulani; Taonani, nditsanulira pa inu mzimu wanga, Ndikudziwitsani mau anga.

24 Cifukwa ndaitana, ndipo munakana; Ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;

25 Koma munapeputsa uphungu wangawonse, Ndi kukana kudzudzula kwanga.

26 Inetu ndidzacitiraciphwete tsoka lanu, Ndidzatonyola pakudza mantha anu;

27 Pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula, Ndi pofika tsoka lanu ngati kabvumvulu; Pakudza kwa inu bvuto ndi nsautso.

28 Pamenepo adzandiitana, koma sindidzabvomera; Adzandifunatu, osandipeza ai;

29 Cifukwa anada nzeru, Sanafuna kuopa Yehova;

30 Anakana uphungu wanga, Nanyoza kudzudzula kwanga konse;

31 Momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao, Nadzakhuta zolingalira zao.

32 Pakuti kubwerera m'mbuyo kwa acibwana kudzawapha; Ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.

33 Koma wondimvera ine adzakhala osatekeseka, Nadzakhala phe osaopa zoipa,

2

1 Mwananga, ukalandira mau anga, Ndi kusunga malamulo anga;

2 Kucherera makutu ako kunzeru, Kulozetsa mtima wako kukuzindikira;

3 Ukaitananso luntha, Ndi kupfuulira kuti ukazindikire;

4 Ukaifunafuna ngati siliva, Ndi kuipwaira ngati cuma cobisika;

5 Pompo udzazindikira kuopa Yehova Ndi kumdziwadi Mulungu.

6 Pakuti Yehova apatsa nzeru; Kudziwa ndi kuzindikira kuturuka m'kamwa mwace;

7 Iye asungira oongoka mtima nzeru yeniyeni; Ndiye cikopa ca oyenda molunjika;

8 Kuti acinjirize njira za ciweruzo, Nadikire khwalala la opatulidwa ace.

9 Pamenepo udzazindikira cilungamo ndi ciweruzo, Zolunjika ndi mayendedwe onse abwino.

10 Pakuti nzeru idzalowa m'mtima mwako, Moyo wako udzakondwera ndi kudziwa,

11 Kulingalira kudzakudikira, Kuzindikira kudzakucinjiriza;

12 Kukupulumutsa ku njira yoipa, Kwa anthu onena zokhota;

13 Akusiya mayendedwe olungama, Akayende m'njira za mdima;

14 Omwe asangalala pocita zoipa, Nakondwera ndi zokhota zoipa;

15 Amene apotoza njira zao, Nakhotetsa mayendedwe ao;

16 Nzeru idzakupulumutsa kwa mkazi waciwerewere, Kwa mkazi wacilendo wosyasyalika ndi mau ace;

17 Wosiya bwenzi la ubwana wace, Naiwala cipangano ca Mulungu wace;

18 Nyumba yace itsikira kuimfa, Ndi mayendedwe ace kwa akufa;

19 Onse akunka kwa iye sabweranso, Safika ku njira za moyo;

20 Nzeru idzakuyendetsa m'njira ya anthu abwino, Kuti usunge mayendedwe a olungama.

21 Pakuti oongoka mtima adzakhala m'dziko, Angwiro nadzatsalamo.

22 Koma oipa adzalikhidwa m'dziko, Aciwembu adzazulidwamo.

3

1 Mwananga, usaiwale malamulo anga, Mtima wako usunge malangizo anga;

2 Pakuti adzakuonjezera masiku ambiri, Ndi zaka za moyo ndi mtendere.

3 Cifundo ndi coonadi zisakusiye; Uzimange pakhosi pako; Uzilembe pamtima pako;

4 Motero udzapezakisomo ndi nzeru yabwino, Pamaso pa Mulungu ndi anthu.

5 Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, Osacirikizika pa luntha lako;

6 Umlemekeze m'njira zako zonse, Ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.

7 Usadziyese wekha wanzeru; Opa Yehova, nupatuke pazoipa;

8 Mitsempha yako idzalandirapo moyo, Ndi mafupa ako uwisi.

9 Lemekeza Yehova ndi cuma cako, Ndi zinthu zako zonse zoyambirira kuca;

10 Motero nkhokwe zako zidzangoti the, Mbiya zako zidzasefuka vinyo.

11 Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova, Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;

12 Pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda; Monga atate mwana amene akondwera naye.

13 Wodala ndi wopeza nzeru, Ndi woona luntha;

14 Pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva, Phindu lace liposa golidi woyengeka.

15 Mtengo wace uposa ngale; Ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.

16 Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lace; Cuma ndi ulemu m'dzanja lace lamanzere.

17 Njira zace ziri zokondweretsa, Mayendedwe ace onse ndiwo mtendere.

18 Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira; Wakulumirira ngwodala.

19 Yehova anakhazika dziko ndi nzeru; Naika zamwamba ndi luntha.

20 Zakuya zinang'ambika ndi kudziwakwace; Thambo ligwetsa mame.

21 Mwananga, zisacokere ku maso ako; Sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;

22 Ndipo mtima wako udzatengapo moyo, Ndi khosi lako cisomo.

23 Pompo udzayenda m'njira yako osaopa, Osapunthwa phazi lako.

24 Ukagona, sudzacita mantha; Udzagona tulo tokondweretsa.

25 Usaope zoopsya zodzidzimutsa, Ngakhale zikadza zopasula oipa;

26 Pakuti Yehova adzalimbitsa mtima wako, Nadzasunga phazi lako lingakodwe.

27 Oyenera kulandira zabwino usawamane; Pokhoza dzanja lako kuwacitira zabwino.

28 Usanene kwa mnzako, Ukabwerenso, Ndipo mawa ndidzakupatsa; Pokhala uli nako kanthu.

29 Usapangire mnzako ciwembu; Popeza akhala nawe pafupi osatekeseka.

30 Usakangane ndi munthu cabe, Ngati sanakucitira coipa,

31 Usacitire nsanje munthu waciwawa; Usasankhe njira yace iri yonse.

32 Pakuti wamphulupulu anyansa Yehova; Koma cinsinsi cace ciri ndi oongoka.

33 Mulungu atemberera za m'nyumba ya woipa; Koma adalitsa mokhalamo olungama.

34 Anyozadi akunyoza, Koma apatsa akufatsa cisomo.

35 Anzeru adzalandira ulemu colowa cao; Koma opusa adzakweza manyazi.

4

1 Ananu, mverani mwambo wa atate, Nimuchere makutu mukadziwe luntha;

2 Pakuti ndikuphunzitsani zabwino; Musasiye cilangizo canga.

3 Pakuti ndinali mwana kwa atate wanga, Wokondedwa ndi mai, ndine ndekha, sanabala wina.

4 Atate nandiphunzitsa, nati kwa ine, Mtima wako uumirire mau anga; Sunga malamulo anga, nukhale ndi moyo.

5 Tenga nzeru, tenga luntha; Usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;

6 Usasiye nzeru, ndipo Idzakusunga; Uikonde, idzakucinjiriza.

7 Nzeru ipambana, tatenga nzeru; M'kutenga kwako konseko utenge luntha.

8 Uilemekeze, ndipo idzakukweza; Idzakutengera ulemu pamene uifungatira.

9 Idzaika cisada ca cisomo pamtu pako; Idzakupatsa korona wokongola.

10 Tamvera mwananga, nulandire mau anga; Ndipo zaka za moyo wako zidzacuruka.

11 Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru, Ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.

12 Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda; Ukathamanga, sudzapunthwa.

13 Gwira mwambo, osauleka; Uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

14 Usalowe m'mayendedwe ocimwa, Usayende m'njira ya oipa.

15 Pewapo, osapitamo; Patukapo, nupitirire.

16 Pakuti akapanda kucita zoipa, samagona; Ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwacokera.

17 Pakuti amadya cakudya ca ucimo, Namwa vinyo wa cifwamba.

18 Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbanda kuca, Kunkabe kuwala kufikira usana woti mbe.

19 Njira ya oipa ikunga mdima; Sadziwa cimene ciwapunthwitsa,

20 Mwananga, tamvera mau anga; Cherera makutu ku zonena zanga.

21 Asacoke ku maso ako; Uwasunge m'kati mwa mtima wako.

22 Pakuti ali moyo kwa omwe awapeza, Nalamitsa thupi lao lonse.

23 Cinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga; Pakuti magwero a moyo aturukamo.

24 Tasiya m'kamwa mokhota, Uike patari milomo yopotoka.

25 Maso ako ayang'ane m'tsogolo, Zikope zako zipenye moongoka,

26 Sinkasinkha bwino mayendedwe a mapazi ako; Njira zako zonse zikonzeke.

27 Usapatuke ku dzanja lamanja kapena kulamanzere; Suntha phazi lako kusiya zoipa.

5

1 Mwananga, mvera nzeru yanga; Cherera makutu ku luntha langa;

2 Ukasunge zolingalira, Milomo yako ilabadire zomwe udziwa.

3 Pakuti milomo ya mkazi waciwerewere ikukha uci; M'kamwa mwace muti see koposa mafuta.

4 Cimariziro cace ncowawa ngati civumulo, Ndi cakuthwa ngati lupanga lakuthwa konse konse.

5 Mayendedwe ace atsikira kuimfa; Mapazi ace aumirira kumanda;

6 Sasinkhasinkha bwino za njira ya moyo; Mayendedwe ace adzandira dzandi dzandi osadziwa iye.

7 Ndipo tsopano ana, mundimvere, Musapatuke ku mau a m'kamwa mwanga.

8 Siyanitsa njira yako kutari kwa iyeyo, Osayandikira ku khomo la nyumba yace;

9 Kuti ungapereke ulemu wako kwa ena, Ndi zaka zako kwa ankhanza;

10 Kuti mphamvu yako isakhutitse alendo, Ndi kuti usagwire nchito m'nyumba ya wacilendo;

11 Ungalire pa cimariziro cako, Pothera nyama yako ndi thupi lako;

12 Ndi kuti, Bwanji ndinada mwambo, Mtima wanga ndi kunyoza cidzudzulo;

13 Ndipo sindinamvera mau a aphunzitsi anga; Ngakhale kucherera makutu kwa akundilanga mwambo!

14 Ndikadakhala m'zoipa zonse, M'kati mwa msonkhano ndi khamu la anthu.

15 Imwa madzi a m'citsime mwako, Ndi madzi oyenda a m'kasupe mwako.

16 Kodi magwero ako ayenera kumwazika kunja, Ndi mitsinje ya madzi m'makwalala?

17 Ikhale ya iwe wekha, Si ya alendo okhala nawe ai.

18 Adalitsike kasupe wako; Ukondwere ndi mkazi wokula nayo.

19 Ngati mbawala yokonda ndi cinkhoma cacisomo, Maere ace akukwanire nthawi zonse; Ukodwe ndi cikondi cace osaleka.

20 Pakuti ukondwerenji, mwananga, ndi mkazi waciwerewere, Ndi kufungatira cifuwa ca mkazi wacilendo?

21 Pakuti njira za munthu ziri pamaso pa Yehova, Asinkhasinkha za mayendedwe ace onse.

22 Zoipazacezacezidzagwira woipa; Adzamangidwa ndi zingwe za ucimo wace.

23 Adzafa posowa mwambo; Adzasocera popusa kwambiri.

6

1 Mwananga, ngati waperekera mnzako cikole, Ngati wapangana kulipirira mlendo,

2 Wakodwa ndi mau a m'kamwa mwako, Wagwidwa ndi mau a m'kamwa mwako.

3 Cita ici tsono; mwananga, nudzipulumutse; Popeza walowa m'dzanja la mnzako, Pita nudzicepetse, numdandaulire mnzako,

4 Usaone tulo m'maso mwako, Ngakhale kuodzera zikope zako.

5 Dzipulumutse wekha ngati mphoyo ku dzanja la msaki, Ndi mbalame ku dzanja la msodzi.

6 Pita kunyerere, wolesi iwe, Penya njira zao nucenjere;

7 Ziribe mfumu, Ngakhale kapitao, ngakhale mkuru;

8 Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe; Nizituta dzinthu zao m'masika.

9 Udzagona mpaka liti, wolesi iwe? Udzauka ku tulo tako liti?

10 Tulo ta pang'ono, kuodzera pang'ono, Kungomanga manja pang'ono, ndi kugona;

11 Ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala, Ndi kusauka kwako ngati munthu wacikopa.

12 Munthu wopanda pace, mwamuna wamphulupulu; Amayenda ndi m'kamwa mokhota;

13 Amatsinzinira ndi maso ace, napalasira ndi mapazi ace, Amalankhula ndi zala zace;

14 Zopotoka ziri m'mtima mwace, amaganizira zoipa osaleka; Amapikisanitsa anthu.

15 Cifukwa cace tsoka lace lidzadza modzidzimuka; Adzasweka msanga msanga, palibe compulumutsa.

16 Ziripo zinthu zisanu ndi cimodzi Mulungu azida; Ngakhale zisanu ndi ziwiri zimnyansa:

17 Maso akunyada, lilime lonama, Ndi manja akupha anthu osacimwa;

18 Mtima woganizira ziwembu zoipa, Mapazi akuthamangira mphulupulu mmangu mmangu;

19 Mboni yonama yonong'ona mabodza, Ndi wopikisanitsa abale.

20 Mwananga, sunga malangizo a atate wako, Usasiye malamulo a mako;

21 Uwamange pamtima pako osaleka; Uwalunze pakhosi pako.

22 Adzakutsogolera ulikuyenda, Ndi kukudikira uli m'tulo, Ndi kulankhula nawe utauka.

23 Pakuti malangizo ndi nyali, malamulo ndi kuunika; Ndi zidzudzulo za mwambo ndizo njira ya moyo;

24 Zikucinjiriza kwa mkazi woipa, Ndi ku lilime losyasyalika la mkazi waciwerewere.

25 Asakucititse kaso m'mtima mwako, Asakukole ndi zikope zace.

26 Pakuti ukayamba ndi mkazi wadama, udzamariza ndi nyenyeswa; Ndipo mkazi wa mwini amasaka moyo wa mtengo wapatari.

27 Kodi mwamuna angatenge moto pa cifuwa cace, Osatentha zobvala zace?

28 Pena kodi mwamuna angayende pa makala oyaka, Osapsya mapazi ace?

29 Comweco wolowa kwa mkazi wa mnzace; Womkhudzayo sadzapulumuka cilango.

30 Anthu sanyoza mbala ikaba, Kuti ikhutitse mtima wace pomva njala;

31 Koma ikapezedwa idzabwezera kasanu ndi kawiri; Idzapereka cuma conse ca m'nyumba yace.

32 Wocita cigololo ndi mkazi alibe nzeru; Wofuna kuononga moyo wace wace ndiye amatero.

33 Adzalasidwa nanyozedwa; Citonzo cace sicidzafafanizidwa.

34 Pakuti nsanje ndiyo ukali wa mwamuna, Ndipo sadzacitira cifundo tsiku lobwezera cilango.

35 Sadzalabadira ciombolo ciri conse, Sadzapembedzeka ngakhale ucurukitsa malipo,

7

1 Mwananga, sunga mau anga, Ukundike malangizo anga;

2 Sunga malangizo anga, nukhale ndi moyo; Ndi malamulo anga ngati mwana wa diso lako.

3 Uwamange pa zala zako, Uwalembe pamtima pako;

4 Nena kwa nzeru, Ndiwe mlongwanga; Nuche luntha mbale wako.

5 Kuti zikucinjirizire kwa mkazi waciwerewere, Kwa mlendo wamkazi wosyasyalika ndi mau ace.

6 Pakuti pa zenera la nyumba yanga Ndinapenyera pa made ace; Ndinaona pakati pa acibwana,

7 Ndinazindikira pakati pa ang'ono Mnyamata wopanda nzeru,

8 Alikupita pakhwalala pafupi ndi mphambano ya pa mkaziyo, Ndi kuyenda pa njira ya ku nyumba yace;

9 Pa madzulo kuli sisiro, Pakati pa usiku pali mdima,

10 Ndipo taona, mkaziyo anamcingamira, Atabvala zadama wocenjera mtima,

11 Ali wolongolola ndi wosaweruzika, Mapazi ace samakhala m'nyumba mwace.

12 Mwina ali kumakwalala, mwina ali kumabwalo, Nabisalira pa mphambano zonse.

13 Ndipo anagwira mnyamatayo, nampsompsona; Nati kwa iye ndi nkhope yacipongwe,

14 Nsembe za mtendere ziri nane; Lero ndacita zowinda zanga.

15 Cifukwa cace ndaturuka kudzakucingamira, Kudzafunitsa nkhope yako, ndipo ndakupeza.

16 Ndayala zopfunda pakama panga, Nsaru zamangamanga za thonje la ku Aigupto,

17 Ndakapiza pamphasa panga mankhwala onunkhira A mvunja ndi cisiyo ndi mtanthanyerere.

18 Tiye tikondwere ndi cikondano mpaka mamawa; Tidzisangalatse ndi ciyanjano.

19 Pakuti mwamuna kulibe kwathu, Wapita ulendo wa kutari;

20 Watenga thumba la ndalama m'dzanja lace, Tsiku lowala mwezi adzabwera kwathu.

21 Amkakamiza ndi kukoka kwa mau ace, Ampatutsa ndi kusyasyalika kwa milomo yace.

22 Mnyamatayo amtsata posacedwa, monga ng'ombe ipita kukaphedwa; Ndi monga unyolo umadza kulanga citsiru;

23 Mpaka mubvi ukapyoza mphafa yace; Amtsata monga mbalame yotamangira msampha; Osadziwa kuti adzaononga moyo wace.

24 Ndipo tsopano, ananga, mundimvere ine, Labadirani mau a m'kamwa mwanga.

25 Mtima wako usapatukire ku njira ya mkaziyo, Usasocere m'mayendedwe ace.

26 Pakuti amagwetsa ambiri, atawalasa; Ndipo ophedwa ndi iye acurukadi.

27 Nyumba yace ndiyo njira ya kumanda, Yotsikira ku zipinda za imfa.

8

1 Kodi nzeru siitana, Luntha ndi kukweza mau ace?

2 Iima pamwamba pa mtunda, Pa mphambano za makwalala;

3 Pambali pa cipata polowera m'mudzi, Polowa anthu pa makomo ipfuula:

4 Ndinu ndikuitanani, amuna, Mau anga ndilankhula kwa ana a anthu.

5 Acibwana inu, cenjerani, Opusa inu, khalani ndi mtima wozindikira;

6 Imvani, pakuti ndikanena zoposa, Ndi zolungama potsegula pakamwa panga,

7 Pakuti m'kamwa mwanga mudzalankhula ntheradi, Zoipa zinyansa milomo yanga.

8 Mau onse a m'kamwa mwanga alungama; Mwa iwo mulibe zokhota ndi zopotoka.

9 Onsewo amveka ndi iye amene azindikira; Alungama kwa akupeza nzeru.

10 Landirani mwambo wanga, si siliva ai; Ndi nzeru kopambana ndi golidi wosankhika.

11 Pakuti nzeru iposa ngale, Ndi zonse tizifunitsa sizilingana nayo,

12 Ine Nzeru ndikhala m'kucenjera, ngati m'nyumba yanga; Ndimapeza kudziwa ndi zolingalira.

13 Kuopa Yehova ndiko kuda zoipa; Kunyada, ndi kudzikuza, ndi njira yoipa, ndi m'kamwa mokhota, ndizida.

14 Ndine mwini uphungu ndi kudziwitsa; Ndine luntha; ndiri ndi mphamvu.

15 Mwa ine mafumu alamulira; Akazembe naweruza molungama.

16 Mwa ine akalonga ayang'anira, Ndi akuru, ngakhale oweruza onse a m'dziko,

17 Akundikonda ndiwakonda; Akundifunafuna adzandipeza.

18 Katundu ndi ulemu ziri ndi ine, Cuma cosatha ndi cilungamo.

19 Cipatso canga ciposa golidi, ngakhale golidi woyengeka; Phindu langa liposa siliva wosankhika.

20 Ndimayenda m'njira ya cilungamo, Pakati pa mayendedwe a ciweruzo,

21 Kuti ndionetse cuma akundikonda, cikhale colowa cao, Ndi kudzaza mosungira mwao.

22 Mulungu anali nane poyamba njira yace, Asanalenge zace zakale.

23 Anandiimika cikhalire ciyambire, Dziko lisanalengedwe.

24 Pamene panalibe zozama ndinabadwa ine, Pamene panalibe akasupe odzala madzi.

25 Mapiri asanakhazikike, Zitunda zisanapangidwe, ndinabadwa;

26 Asanalenge dziko, ndi thengo, Ngakhale ciyambi ca pfumbi la dziko.

27 Pamene anakhazika mlengalenga ndinali pompo; Pamene analemba pazozama kwete kwete;

28 Polimbitsa Iye thambo la kumwamba, Pokula akasupe a zozama.

29 Poikira nyanja malire ace, Kuti madzi asapitirire pa lamulo lace; Polemba maziko a dziko,

30 Ndinali pa mbali pace ngati mmisiri; Ndinamsekeretsa tsiku ndi tsiku, Ndi kukondwera pamaso pace nthawi zonse;

31 Ndi kukondwera ndi dziko lace lokhalamo anthu, Ndi kusekerera ndi ana a anthu.

32 Ndipo tsopano, ananga, mundimvere ine, Ngodala akusunga njira zanga.

33 Imvani mwambo, mukhale anzeru osaukana.

34 Ngwodala amene andimvera, nadikira pa zitseko zanga tsiku ndi tsiku, Ndi kulinda pa mphuthu za makoma anga;

35 Pakuti wondipeza ine apeza moyo; Yehova adzamkomera mnma.

36 Koma wondicimwira apweteka moyo wace; Onse akundida ine akonda imfa.

9

1 Nzeru yamanga nyumba yace, Yasema zoimiritsa zace zisanu ndi ziwiri;

2 Yaphera nyama yace, nisanganiza vinyo wace, Nilongosolanso pa gome lace.

3 Yatuma anamwali ace, iitana Pa misanje ya m'mudzi.

4 Wacibwana yense apambukire kuno; Iti kwa yense wosowa nzeru,

5 Tiyeni, idyani cakudya canga; Nimumwe vinyo wanga ndamsanganiza.

6 Lekani, acibwana inu, nimukhale ndi moyo; Nimuyende m'njira ya nzeru.

7 Woweruza munthu wonyoza adzicititsa yekha manyazi; Yemwe adzudzula wocimwa angodetsa mbiri yace yace.

8 Usadzudzule wonyoza kuti angakude; Dzudzula wanzeru adzakukonda.

9 Ukacenjeza wanzeru adzakulitsa nzeru yace; Ukaphunzitsa wolungama adzaonjezera kuphunzira,

10 Ciyambi ca nzeru ndico kuopa Yehova; Kudziwa Woyerayo ndiko luntha;

11 Pakuti mwa ine masiku ako adzacuruka, Zaka za moyo wako zidzaonjezedwa.

12 Ukakhala wanzeru, si yako yako nzeruyo? Ndipo ukanyoza udzasauka wekha.

13 Utsiru umalongolola, Ngwa cibwana osadziwa kanthu.

14 Ukhala pa khomo la nyumba yace, Pampando pa misanje ya m'mudzi

15 Kuti uitane akupita panjira, Amene angonkabe m'kuyenda kwao,

16 Wacibwana ndani? Apambukire kuno. Ati kwa yense wopanda nzeru,

17 Madzi akuba atsekemera, Ndi cakudya cobisika cikoma.

18 Ndipo mwamunayo sadziwa kuti akufa ali konko; Omwe acezetsa utsiru ali m'manda akuya.

10

1 Mwana wanzeru akondweretsa atate; Koma mwana wopusa amvetsa amace cisoni.

2 Cuma ca ucimo sicithangata: Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.

3 Yehova samvetsa njala moyo wa wolungama; Koma amainga cifuniro ca wocimwa.

4 Wocita ndi dzanja laulesi amasauka; Koma dzanja la akhama lilemeretsa.

5 Wokolola m'malimwe ndi mwana wanzeru; Koma wogona pakututa ndi mwana wocititsa manyazi.

6 Madalitso ali pamtu pa wolungama Koma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.

7 Amayesa wolungama wodala pamkumbukira; Koma dzina la oipa lidzabvunda.

8 Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo; Koma citsiru colongolola cidzagwa.

9 Woyenda moongoka amayenda osatekeseka; Koma wokhotetsa njira zace adzadziwika.

10 Wotsinzinira acititsa cisoni; Koma wodzudzula momveka acita mtendere.

11 M'kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo; Koma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.

12 Udani upikisanitsa; Koma cikondi cikwirira zolakwa zonse.

13 Nzeru ipezedwa m'milomo ya wozindikira; Koma wopusa pamsana pace ntyole.

14 Anzeru akundika zomwe adziwa Koma m'kamwa mwa citsiru muononga tsopano lino.

15 Cuma ca wolemera ndi mudzi wace wolimba; Koma umphawi wao uononga osauka.

16 Nchito za wolungama zipatsa moyo; Koma phindu la oipa licimwitsa.

17 Wosunga mwambo ali m'njira ya moyo; Koma wosiya cidzudzulo asocera.

18 Wobisa udani ali ndi milomo yonama; Wonena ugogodi ndiye citsiru.

19 Pocuruka mau zolakwa sizisoweka; Koma wokhala cete acita mwanzeru.

20 Lilime la wolungama likunga siliva wosankhika; Koma mtima wa oipa uli wacabe.

21 Milomo ya wolungama imadyetsa ambiri; Koma zitsiru zimafa posowa nzeru.

22 Madalitso a Yehova alemeretsa, Saonjezerapo cisoni.

23 Masewero a citsiru ndiwo kucita zoipa; Koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.

24 Comwe woipa aciopa cidzamfikira; Koma comwe olungama acifuna cidzapatsidwa.

25 Monga kabvumvulu angopita, momwemo woipa kuti zi; Koma olungama ndiwo maziko osatha.

26 Ngati vinyo wowawa m'mano, ndi utsi m'maso, Momwemo wolesi kwa iwo amene amtuma.

27 Kuopa Yehova kutanimphitsa masiku; Koma zaka za oipa zidzafinimpha,

28 Ciyembekezo ca olungama ndico cimwemwe; Koma cidikiro ca oipa cidzaonongeka.

29 Njira ya Yehova ndi linga kwa woongoka mtima; Koma akucita zoipa adzaonongeka.

30 Wolungama sadzacotsedwa konse: Koma oipa sadzakhalabe m'dziko.

31 M'kamwa mwa wolungama mulankhula nzeru; Koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32 Milomo ya wolungama idziwa zokondweretsa; Koma m'kamwa mwa oipa munena zokhota,

11

1 Muyeso wonyenga unyansa Yehova; Koma mulingo wamphumphu umsekeretsa.

2 Pakudza kudzikuza padzanso manyazi; Koma nzeru iri ndi odzicepetsa,

3 Kuongoka mtima kwa olungama kuwatsogolera; Koma kukhota kwa aciwembu kudzawaononga.

4 Cuma sicithandiza tsiku la mkwiyo; Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.

5 Cilungamo ca wangwiro cimaongola njira yace; Koma woipa adzagwa ndi zoipa zace.

6 Cilungamo ca oongoka mtima cidzawapulumutsa; Koma aciwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.

7 Pomwalira woipa cidikiro cace cionongeka; Ciyembekezo ca ucimo cionongeka.

8 Wolungama apulumuka kubvuto; Woipa nalowa m'malo mwace.

9 Wonyoza Mulungu aononga mnzace ndi m'kamwa mwace; Koma olungama adzapulumuka pakudziwa,

10 Olungama akapeza bwino, mudzi usekera; Nupfuula pakuonongeka oipa.

11 Madalitso a olungama akuza mudzi; Koma m'kamwa mwa oipa muupasula.

12 Wopeputsa mnzace asowa nzeru; Koma wozindikira amatonthola.

13 Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi; Koma wokhulupirika mtima abisa mau.

14 Popanda upo wanzeru anthu amagwa; Koma pocuruka aphungu pali cipulumutso.

15 Woperekera mlendo cikole adzaphwetekwapo; Koma wakuda cikole akhala ndi mtendere.

16 Mkazi wodekha agwiritsa ulemu; Aukali nagwiritsa cuma.

17 Wacifundo acitira moyo wace zokoma; Koma wankhanza abvuta nyama yace.

18 Woipa alandira malipiro onyenga; Koma wofesa cilungamo aonadi mphotho,

19 Wolimbikira cilungamo alandira moyo; Koma wolondola zoipa adzipha yekha,

20 Okhota mtima anyansa Yehova; Koma angwiro m'njira zao amsekeretsa.

21 Zoonadi, wocimwa sadzapulumuka cilango; Koma mbeu ya olungama idzalanditsidwa.

22 Monga cipini cagolidi m'mphuno ya nkhumba, Momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.

23 Cifuniro ca olungama cifikitsa zabwino zokha; Koma ciyembekezo ca oipa mkwiyo.

24 Alipo wogawira, nangolemerabe; Aliponso womana comwe ayenera kupatsa nangosauka.

25 Mtima wa mataya udzalemera; Wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.

26 Womana tirigu anthu amtemberera; Koma madalitso adzakhala pamtu pa wogulitsa.

27 Wopwaira ubwino afunitsa cikondwerero; Koma zoipa zidzamfikira wozilondola.

28 Wokhulupmra cuma cace adzagwa; Koma olungama adzaphuka ngati tsamba.

29 Wobvuta banja lace adzalowa m'zomsautsa; Wopusa adzatumikira wanzeru.

30 Cipatso ca wolungama ndi mtengo wa moyo; Ndipo wokola mtima ali wanzeru.

31 Taonani, wolungama adzalandira mphotho kunja kuno; Koposa kotani woipa ndi wocimwa?

12

1 Wokonda mwambo akonda kudziwa; Koma wakuda cidzudzulo apulukira.

2 Yehova akomera mtima munthu wabwino; Koma munthu wa ziwembu amtsutsa,

3 Munthu sadzakhazikika ndi udio, Muzu wa olungama sudzasunthidwa.

4 Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wace; Koma wocititsa manyazi akunga cobvunditsa mafupa a mwamunayo.

5 Maganizo a olungama ndi ciweruzo; Koma uphungu wa oipa unyenga.

6 Mau a oipa abisalira mwazi; Koma m'kamwa mwa olungama muwalanditsa.

7 Oipa amagwa kuli zi; Koma banja la olungama limaimabe.

8 Munthu amatamandidwa monga mwa nzeru yace; Koma wokhota mtima adzanyozedwa.

9 Wonyozedwa, amene ali ndi kapolo, Aposa wodzikuza, amene asowa zakudya.

10 Wolungama asamalira moyo wa coweta cace; Koma cifundo ca oipa ndi nkhanza.

11 Zakudyazikwanira wolima minda yace; Koma wotsata anthu opanda pace asowa nzeru.

12 Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu; Koma muzu wa olungama umabala zipatso.

13 M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa; Koma wolungama amaturuka m'mabvuto.

14 Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace; Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.

15 Njira ya citsiru nlolungama pamaso pace pace; Koma wanzeru amamvera uphungu.

16 Mkwiyo wa citsiru udziwika posacedwa; Koma wanzeru amabisa manyazi.

17 Wolankhula ntheradi aonetsa cilungamo; Koma mboni yonama imanyenga.

18 Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga; Koma lilime la anzeru lilamitsa.

19 Mlomo wa ntheradi ukhazikika nthawi zonse; Koma lilime lonama likhala kamphindi.

20 Cinyengo ciri m'mitima ya oganizira zoipa; Koma aphungu a mtendere amakondwa.

21 Palibe bvuto lidzagwera wolungama; Koma amphulupulu adzadzazidwa ndi zoipa,

22 Milomo yonama inyansa Yehova; Koma ocita ntheradi amsekeretsa.

23 Munthu wanzeru abisa zomwe adziwa; Koma mtima wa opusa ulalikira utsiru.

24 Dzanja la akhama lidzalamulira; Koma wolesi adzakhala ngati kapolo,

25 Nkhawa iweramitsa mtima wa munthu; Koma mau abwino aukondweretsa.

26 Wolungama atsogolera mnzace; Koma njira ya oipa iwasokeretsa.

27 Wolesi samaocha nyama yace anaigwira; Koma wolungama amalandira cuma copambana ca anthu.

28 M'khwalala la cilungamo muli moyo; M'njira ya mayendedwe ace mulibe imfa.

13

1 Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate; Koma wonyoza samvera cidzudzulo.

2 Munthu adzadya zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace; Koma moyo wa aciwembu udzadya ciwawa.

3 Wogwira pakamwa pace asunga moyo wace; Koma woyasamula milomo yace adzaonongeka.

4 Moyo wa wolesi ukhumba osalandira kanthu; Koma moyo wa akhama udzalemera.

5 Wolungama ada mau onama; Koma woipa anyansa, nadzicititsa manyazi,

6 Cilungamo cicinjiriza woongoka m'njira; Koma udio ugwetsa wocimwa.

7 Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu; Alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi cuma cambiri.

8 Ciombolo ca moyo wa munthu ndico cuma cace; Koma wosauka samva cidzudzulo.

9 Kuunika kwa olungama kukondwa; Koma nyali ya oipa idzazima.

10 Kudzikuza kupikisanitsa; Koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

11 Cuma colandiridwa mokangaza cidzacepa; Koma wokundika ndi dzanja adzaona zocuruka.

12 Ciyembekezo cozengereza cidwalitsa mtima; Koma pakufika cifuniroco ndico mtengo wa moyo.

13 Wonyoza mau adziononga yekha; Koma woopa malangizo adzalandira mphotho.

14 Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo, Apatutsa ku misampha ya imfa.

15 Nzeru yabwino ipatsa cisomo; Koma njira ya aciwembu iri makolokoto.

16 Yense wocenjera amacita mwanzeru: Koma wopusa aonetsa utsiru.

17 Mthenga wolakwa umagwa m'zoipa; Koma mtumiki wokhulupirika alamitsa.

18 Wokana mwambo adzasauka nanyozedwa; Koma wolabadira cidzudzulo adzalemekezedwa.

19 Cifuniro cikondweretsa moyo citacitidwa; Koma kusiya zoipa kunyansa opusa,

20 Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru: Koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

21 Zoipa zilondola ocimwa; Koma olungama adzalandira mphotho yabwino.

22 Wabwino asiyira zidzukulu zace colowa cabwino; Koma wocimwa angosungira wolungama cuma cace.

23 M'kulima kwa osauka muli zakudya zambiri; Koma zinazo zimaonongeka posowa ciweruzo.

24 Wolekereramwanace osammenya amuda; Koma womkonda amyambize kumlanga.

25 Wolungama adya nakhutitsa moyo wace; Koma mimba ya oipa idzasowa.

14

1 Mkazi yense wanzeru amanga banja lace; Koma wopusa alipasula ndi manja ace.

2 Woyenda moongoka mtima aopa Yehova; Koma wokhota m'njira yace amnyoza,

3 M'kamwa mwa citsiru muli ntyole ya kudzikuza; Koma milomo ya anzeru Idzawasunga.

4 Popanda zoweta modyera muti see; Koma mphamvu ya ng'ombe icurukitsa phindu.

5 Mboni yokhulupirika sidzanama; Koma mboni yonyenga imalankhula zonama.

6 Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza; Koma wozindikira saona bvuto m'kuphunzira.

7 Pita pamaso pa munthu wopusa, Sudzazindikira milomo yakudziwa.

8 Nzeru ya wocenjera ndiyo yakuti azindikire njira yace; Koma utsiru wa opusa ndiwo cinyengo.

9 Zitsiru zinyoza kuparamula; Koma mwa oongoka mtima muli ciyanjano.

10 Mtima udziwa kuwawa kwace kwace; Mlendo sadudukira ndi cimwemwe cace.

11 Nyumba ya oipa idzapasuka; Koma hema wa oongoka mtima adzakula.

12 Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka; Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.

13 Ngakhale m'kuseka mtima uwawa; Ndipo matsiriziro a ciphwete ndi cisoni.

14 Wobwerera m'mbuyo m'mtima adzakhuta njira zace; Koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.

15 Wacibwana akhulupirira mau onse; Koma wocenjera asamalira mayendedwe ace.

16 Wanzeru amaopa nasiya zoipa; Koma wopusa amanyada osatekeseka.

17 Wokangaza kukwiya adzacita utsiru; Ndipo munthu wa ziwembu adzadedwa.

18 Acibwana amalandira colowa ca utsiru; Koma ocenjera amabvala nzeru ngati korona.

19 Oipa amagwadira abwino, Ndi ocimwa pa makomo a olungama.

20 Waumphawi adedwa ndi anzace omwe; Koma akukonda wolemera acuruka.

21 Wonyoza anzace acimwa; Koma wocitira osauka cifundo adala.

22 Kodi oganizira zoipa sasocera? Koma akuganizira zabwino adzalandira cifundo ndi ntheradi.

23 M'nchito zonse muli phindu; Koma kulankhula-lankhula kungopatsa umphawi.

24 Korona wa anzeru ndi cuma cao; Utsiru wa opusa ndiwo utsiru.

25 Mboni yoona imalanditsa miyoyo; Koma wolankhula zonama angonyenga.

26 Wakuopa Yehova akhulupirira kolimba; Ndipo ana ace adzakhala ndi pothawirapo.

27 Kuopa Yehova ndiko kasupe wa moyo, Kupatutsa ku misampha ya imfa.

28 Mu unyinji wa anthu muli ulemu wa mfumu; Koma popanda anthu kalonga aonongeka.

29 Wosakwiya msanga apambana kumvetsa; Koma wansontho akuza utsiru.

30 Mtima wabwino ndi moyo wa thupi; Koma nsanje ibvunditsa mafupa.

31 Wotsendereza aumphawi atonza Mlengi wace; Koma wocitira wosauka cifundo amlemekeza.

32 Wocimwa adzakankhidwa m'kuipa kwace; Koma wolungama akhulupirirabe pomwalira,

33 Nzeru ikhalabe m'mtima wa wozindikira, Nidziwika pakati pa opusa.

34 Cilungamo cikuza mtundu wa anthu; Koma cimo licititsa pfuko manyazi.

35 Mfumu ikomera mtima kapolo wocita mwanzeru; Koma idzakwiyira wocititsa manyazi.

15

1 Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo; Koma mau owawitsa aputa msunamo.

2 Lilime la anzeru linena bwino zomwe adziwa; Koma m'kamwa mwa opusa mutsanulira utsiru.

3 Maso a Yehova ali ponseponse, Nayang'anira oipa ndi abwino.

4 Kuciza lilime ndiko mtengo wa moyo; Koma likakhota liswa moyo.

5 Citsiru cipeputsa mwambo wa atate wace; Koma wosamalira cidzudzulo amacenjera.

6 M'nyumba ya wolungama muli katundu wambiri; Koma m'phindu la woipa muli bvuto,

7 Milomo ya anzeru iwanditsa nzeru, Koma mtima wa opusa suli wolungama.

8 Nsembe ya oipa inyansa Yehova; Koma pemphero la oongoka mtima limkondweretsa.

9 Njira ya oipa inyansa Yehova; Koma akonda wolondola cilungamo.

10 Wosiya njira adzalangidwa mowawa; Wakuda cidzudzulo adzafa.

11 Kumanda ndi kucionongeko kuli pamaso pa Yehova; Koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?

12 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa, Samapita kwa anzeru.

13 Mtima wokondwa usekeretsa nkhope; Koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.

14 Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa; Koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.

15 Masiku onse a wosauka ali oipa; Koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.

16 Zapang'ono, ulikuopa Yehova, Zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso,

17 Kudya masamba, pali cikondano, Kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.

18 Munthu wozaza aputa makani; Koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.

19 Mayendedwe a wolesi akunga Hnga laminga, Koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.

20 Mwana wanzeru akondweretsa atate wace; Koma munthu wopusa apeputsa amace.

21 Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru; Koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ace.

22 Zolingalira zizimidwa popanda upo Koma pocuruka aphungu zikhazikika.

23 Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwace; Ndi mau a pa nthawi yace kodi sali abwino?

24 Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera, Kuti apambuke kusiya kunsi kwa manda.

25 Yehova adzapasula nyumba ya wonyada; Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,

26 Ziwembu zoipa zinyansa Yehova; Koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.

27 Wopindula monyenga abvuta nyumba yace; Koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.

28 Mtima wa wolungama uganizira za mayankhidwe; Koma m'kamwa mwa ocimwa mutsanulira zoipa.

29 Yehova atarikira oipa; Koma pemphero la olungama alimvera.

30 Kuunika kwa maso kukondweretsa mtima; Ndipo pomveka zabwino mafupa amatenga uwisi.

31 Khutu lomvera cidzudzulo ca moyo Lidzakhalabe mwa anzeru.

32 Wokana mwambo apeputsa moyo wace; Koma wosamalira cidzudzulo amatenga nzeru.

33 Kuopa Yehova ndiko mwambo wanzeru; Ndipo cifatso citsogolera ulemu.

16

1 Malongosoledwe a mtima nga munthu; Koma mayankhidwe a lilime acokera kwa Yehova.

2 Njira zonse za munthu ziyera pamaso pace; Koma Yehova ayesa mizimu.

3 Pereka zocita zako kwa Yehova, Ndipo zolingalira zako zidzakhazikika.

4 Zonse Yehova anazipangaziri ndi zifukwa zao; Ngakhale amphulupulu kuti aone tsiku loipa,

5 Yense wonyada mtima anyansa Yehova; Zoonadi sadzapulumuka cilango.

6 Mphulupulu iomboledwa ndi cifundo ndi ntheradi; Apatuka pa zoipa poopa Yehova.

7 Njira za munthu zikakonda Yehova, Ayanjanitsana naye ngakhale adani ace.

8 Zapang'ono, pokhala cilungamo, Ziposa phindu lalikuru lopanda ciweruzo.

9 Mtima wa munthu ulingalira njira yace; Koma Yehova ayendetsa mapazi ace.

10 Mau a mlauli ali m'milomo ya mfumu; M'kamwa mwace simudzacita cetera poweruza.

11 Mwini muyeso ndi mulingo wolungama ndiye Yehova; Ndiyenso anapanga miyala yonse yoyesera ya m'thumba.

12 Kucita mphulupulu kunyansa mafumu; Pakuti mpando wao wakhazikika ndi cilungamo.

13 Milomo yolungama ikondweretsa mafumu; Wonena zoongoka amkonda.

14 Mkwiyo wa mfumu ndi mithenga ya imfa; Wanzeru adzaukhulula.

15 M'kuunika kwa nkhope ya mfumu muli moyo; Kukoma mtima kwace kunga mtambo wa mvula ya masika.

16 Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golidi, Kulandira luntha ndi kusankhika koposa siliva?

17 Khwalala la oongoka mtima ndilo lakuti asiye zoipa; Wosunga njira yace acinjiriza moyo wace.

18 Kunyada kutsogolera kuonongeka Mtinia wodzikuza ndi kutsogolera kupunthwa.

19 Kufatsa mtima ndi osauka Kuposa kugawana zofunkha ndi onyada.

20 Wolabadira mau adzapeza bwino; Ndipo wokhulupirira Yehova adala.

21 Wanzeru mtima adzachedwa wocenjera; Ndipo kukoma kwa milomo kuyenjezera kuphunzira.

22 Nzeru ndi kasupe wa moyo kwa mwini wace; Koma mwambo wa zitsiru ndi utsiru.

23 Mtima wa wanzeru ucenjeza m'kamwa mwace, Nuphunzitsanso milomo yace.

24 Mau okoma ndiwo cisa ca uci, Otsekemera m'moyo ndi olamitsa mafupa.

25 Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka, Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.

26 Wanchito adzigwirira yekha nchito; Pakuti m'kamwa mwace mumfulumiza.

27 Munthu wopanda pace akonzeratu zoipa; Ndipo m'milomo mwace muli moto wopsereza.

28 Munthu wokhota amautsa makani; Kazitape afetsa ubwenzi.

29 Munthu waciwawa akopa mnzace, Namuyendetsa m'njira yosakhala bwino.

30 Wotsinzina ndiye aganizira zakhota; Wosunama afikitsa zoipa.

31 Imvi ndiyo korona wa ulemu, Idzapezedwa m'njira ya cilungamo.

32 Wosakwiya msanga aposa wamphamvu; Wolamulira mtima wace naposa wolanda mudzi.

33 Maere aponyedwa pamfunga; Koma ndiye Yehova alongosola zonse.

17

1 Nyenyeswa youma, pokhala mtendere, Iposa nyumba yodzala nyama yansembe, pali makangano.

2 Kapolo wocitamwanzeru Adzalamulira mwana wocititsa manyazi, Nadzagawana nao abale colowa.

3 Siliva ali ndi mbiya yosungunulira, golidi ali ndi ng'anjo; Koma Yehova ayesa mitima.

4 Wocimwa amasamalira milomo yolakwa; Wonama amvera lilime losakaza.

5 Wocitira ciphwete aumphawi atonza Mlengi; Wokondwera ndi tsoka sadzapulumuka cilango.

6 Zidzukulu ndizo korona wa okalamba; Ndipo ulemerero wa ana ndiwo atate ao.

7 Mlomo wangwiro suyenera citsiru; Ngakhale mlomo wonama suyenera kalonga ndi pang'ono ponse.

8 Wolandira cokometsera mlandu aciyesa ngale; Pali ponse popita iye acenjera.

9 Wobisa colakwa afunitsa cikondano; Koma wobwereza-bwereza mau afetsa ubwenzi.

10 Cidzudzulo cilowa m'kati mwa wozindikira, Kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.

11 Woipa amafuna kupanduka kokha; Koma adzamtumizira mthenga wankhanza.

12 Kukomana ndi citsiru m'kupusa kwace Kuopsya koposa cirombo cocicotsera anace.

13 Wobwezera zabwino zoipa, Zoipa sizidzamcokera kwao.

14 Ciyambi ca ndeu cifanana ndi kutsegulira madzi; Tsono kupikisana kusanayambe tasiya makani.

15 Wokometsa mlandu wa wamphulupulu, ndi wotsutsa wolungama, Onse awiriwa amnyansa Yehova.

16 Kodi bwanji mtengo wogulira nzeru uli m'dzanja la citsiru, Popeza wopusa alibe mtima?

17 Bwenzi limakonda nthawi zonse; Ndipo mbale anabadwira kuti akuthandize pooneka tsoka.

18 Munthu wosowa nzeru apangana kulipirira wina, Napereka cikole pamaso pa mnzace.

19 Wokonda ndeu akonda kulakwa; Ndipo wotarikitsa khomo lace afunafuna kuonongeka.

20 Wokhota mtima sadzapeza bwino Ndipo mwini lilime lokhota adzagwa m'zoipa.

21 Wobala citsiru adzicititsa cisoni; Ndipo atate wa wopusa sakondwa.

22 Mtima wosekerera uciritsa bwino Koma mzimu wosweka uphwetsa mafupa,

23 Munthu woipa alandira cokometsera mlandu coturutsa m'mfunga, Kuti apambukitse mayendedwe a ciweruzo.

24 Nzeru iri pamaso pa wozindikira; Koma maso a wopusa ali m'malekezero a dziko.

25 Mwana wopusa acititsa atate wace cisoni, Namvetsa zowawa amace wombala.

26 Kulipiritsa wolungama sikuli kwabwino, Ngakhale kukwapula akuru cifukwa aongoka mtima.

27 Wopanda cikamwakamwa apambana kudziwa; Ndipo wofatsa mtima ali wanzeru.

28 Ngakhalecitsirucikatontholaaciyesa canzeru; Posunama ali wocenjera.

18

1 Wopanduka afunafuna niro cace, Nakangana ndi nzeru yonse yeniyeni.

2 Wopusa sakondwera ndi kuzindikira; Koma kungobvumbulutsa za m'mtima mwace.

3 Pakudza wamphulupulu padzanso kunyoza; Manyazi natsagana ndi citonzo.

4 Mau a m'kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya; Kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.

5 Kukometsa mlandu wa wamphulupulu mwatsankhu sikuli kwabwino, Ngakhale kucitira cetera wolungama.

6 Milomo ya wopusa ifikitsa makangano; Ndipo m'kamwa mwace muputa kukwapulidwa.

7 M'kamwa mwa wopusa mumuononga, Milomo yace ikhala msampha wa moyo wace.

8 Mau a kazitape akunga zakudya zolongosoka, Zotsikira m'kati mwa mimba.

9 Wogwira nchito mwaulesi Ndiye mbale wace wa wosakaza.

10 Dzina la Yehova ndilo linga lolimba; Wolungama athamangiramo napulumuka.

11 Cuma ca wolemera ndico mudzi wace wolimba; Alingalira kuti ndico khoma lalitari.

12 Mtima wa munthu unyada asanaonongeke; Koma cifatso citsogolera ulemu.

13 Wobwezera mau asanamvetse apusa, Nadzicititsa manyazi.

14 Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala; Koma ndani angatukule mtima wosweka?

15 Mtima wa wozindikira umaphunzira; Khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.

16 Mtulo wa munthu umtsegulira njira, Numfikitsa pamaso pa akuru.

17 Woyamba kudzinenera ayang'anika wolungama; Koma mnzace afika namuululitsa zace zonse.

18 Ula uletsa makangano, Nulekanitsa amphamvu.

19 Kupembedza mbale utamcimwira nkobvuta, Kulanda mudzi wolimba nkosabvuta; Makangano akunga mipiringidzo ya linga.

20 Mimba ya munthu idzakhuta zipatso za m'kamwa mwace; Iye nadzakhuta phindu la milomo yace.

21 Lilime liri ndi mphamvu pa imfa ndi moyo; Wolikonda adzadya zipatso zace.

22 Wopeza mkazi apeza cinthu cabwino; Yehova amkomera mtima.

23 Wosauka amadandaulira; Koma wolemera ayankha mwaukali.

24 Woyanjana ndi ambiri angodziononga; Koma liripo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.

19

1 Wosauka woyenda mwangwiro Aposa wokhetsa milomo ndi wopusa.

2 Kukhumba kosadziwa sikuli kwabwino; Ndipo wofulumira ndi mapazi ace amacimwa.

3 Utsiru wa munthu ukhotetsa njira yace; Mtima wace udandaula pa Yehova.

4 Cuma cionjezetsa mabwenzi ambiri; Koma mnzace wa waumphawi amleka.

5 Mboni yonama sidzakhala yosalangidwa; Wolankhula mabodza sadzapulumuka.

6 Ambiri adzapembedza waufulu; Ndipo yense ndi bwenzi la munthu wopatsa.

7 Abale onse a wosauka amuda; Nanga mabwenzi ace kodi satanimphirana naye? Awatsata ndi mau, koma kuli zi.

8 Wolandira nzeru akonda moyo wace; Wosunga luntha adzapeza zabwino.

9 Mboni yonama sidzapulumuka cilango; Wolankhula mabodza adzaonongeka.

10 Wopusa sayenera kukhala ndi zinthu zolongosoka; Nanga kapolo ayenera kulamulira akalonga kodi?

11 Kulingalira kwa munthu kucedwetsa mkwiyo; Ulemerero wace uli wakuti akhululukire colakwa.

12 Mkwiyo wa mfumu ukunga kubangula kwa mkango; Koma kukoma mtima kwace kunga mame pamsipu.

13 Mwana wopusa ndiye tsoka la atate wace; Ndipo makangano a mkazi ndiwo kudontha-donthabe.

14 Nyumba ndi cuma ndizo colowa ca atate; Koma mkazi wanzeru acokera kwa Yehova.

15 Ulesi ugonetsa tulo tofa nato; Ndipo moyo wamkhongono udzamva njala.

16 Wosunga lamulo asunga moyo wace; Wonyalanyaza mayendedwe ace adzafa.

17 Wocitira waumphawi cifundo abwereka Yehova; Adzambwezera cokoma caceco.

18 Menya mwanako, ciyembekezero ciripo, Osafunitsa kumuononga.

19 Munthu waukali alipire mwini; Pakuti ukampulumutsa udzateronso.

20 Tamvera uphungu, nulandire mwambo, Kuti ukhale wanzeru pa cimariziro cako,

21 Muli zolingalira zambiri m'mtima mwa munthu; Koma uphungu wa Yehova ndiwo udzaimika.

22 Cotikondetsa munthu ndico kukoma mtima kwace; Ndipo wosauka apambana munthu wonama.

23 Kuopa Yehova kupatsa moyo; Wokhala nako adzakhala wokhuta; Zoipa sizidzamgwera.

24 Wolesi alonga dzanja lace m'mbale, Osalibwezanso kukamwa kwace.

25 Menya wonyoza, ndipo acibwana adzaceniera; Nudzudzule wozindikira adzazindikira nzeru.

26 Wolanda za atate, ndi wopitikitsa amai, Ndiye mwana wocititsa manyazi ndi wogwetsa nkhope.

27 Ukangofuna, mwananga, kusocera kusiya mau akudziwitsa, Leka kumva mwambo.

28 Mboni yopanda pace inyoza ciweruzo; M'kamwa mwa amphulupulu mumeza zoipa,

29 Akonzera onyoza ciweruzo, Ndi mikwingwirima pamsana pa opusa.

20

1 Vinyo acita ciphwete, cakumwa caukali cisokosa; Wosocera nazo alibe nzeru.

2 Kuopsya kwa mfumu ndiko kubangula kwa mkango; Womputa acimwira moyo wace wace.

3 Kuli ulemu kwa mwamuna kupewa ndeu; Koma zitsiru zonse zimangokangana,

4 Wolesi salima cifukwa ca cisanu; Adzapemphapempha m'masika osalandira kanthu.

5 Uphungu wa m'mtima mwa munthu ndiwo madzi akuya; Koma munthu wozindikira adzatungapo,

6 Anthu ambiri abukitsa yense kukoma mtima kwace; Koma ndani angapeze munthu wokhulupirika?

7 Wolungama woyenda mwangwiro, Anace adala pambuyo pace.

8 Mfumu yokhala pa mpando waweruzira Ipitikitsa zoipa zonse ndi maso ace.

9 Ndani anganene, Ndasambitsa mtima wanga, Ndayera opanda cimo?

10 Miyeso yosiyana, ndi malicero osiyana, Zonse ziwirizi zinyansa Yehova.

11 Ngakhale mwana adziwika ndi nchito zace; Ngati nchito yace iri yoyera ngakhale yolungama.

12 Khutu lakumva, ndi diso lopenya, Yehova anapanga onse awiriwo.

13 Usakonde tulo ungasauke; Phenyula maso, udzakhuta zakudya.

14 Wogula ati, Cacabe cimeneco. Koma atacoka adzitama.

15 Alipo golidi ndi ngale zambiri; Koma milomo yodziwa ndiyo cokometsera ca mtengo wapatari.

16 Tenga maraya a woperekera mlendo cikole; Woperekera mkazi wacilendo cikole umgwire mwini.

17 Zakudya za cinyengo zikondweretsa munthu; Koma pambuyo pace m'kamwa mwace mudzadzala tinsangalabwi.

18 Uphungu utsimikiza zolingalira, Ponya nkhondo utapanga upo.

19 Kazitape woyendayenda awanditsa zinsinsi; Usadudukire woyasama milomo yace.

20 Wotemberera atate wace ndi, amace, Nyali yace idzazima mu mdima woti bi.

21 Colowa cingalandiridwe msanga msanga poyamba pace; Koma citsiriziro cace sicidzadala.

22 Usanene, Ndidzabwezera zoipa; Yembekeza Yehova, adzakupulumutsa.

23 Miyeso yosiyana inyansa Yehova, Ndi mulingo wonyenga suli wabwino.

24 Yehova alongosola mayendedwe a mwamuna; Munthu tsono angazindikire bwanji njira yace?

25 Kunena mwansontho, ici ncopatulika, kuli msampha kwa munthu, Ndi kusinkhasinkha pambuyo pace atawinda.

26 Mfumu yanzeru ipeta amphulupulu, Niyendetsapo njinga ya gareta.

27 Mzimu wa munthu ndiwo nyali ya Yehova; Usanthula m'kati monse mwa mimba.

28 Cifundo ndi ntheradi zisunga mfumu; Cifundo cicirikiza mpando wace.

29 Ulemerero wa anyamata ndiwo mphamvu yao; Kukongola kwa nkhalamba ndi

30 Mikwingwirima yopweteka icotsa zoipa; Ndi mikwapulo ilowa m'kati mwa mimba.

21

1 Mtima wa mfumu uli m'dzanja la Yehova ngati mitsinje ya madzi; Aulozetsa komwe afuna.

2 Njira zonse za munthu zilungama pamaso pace; Koma Yehova ayesa mitima.

3 Kucita cilungamo ndi ciweruzo Kupambana ndi nsembe kumkonda Yehova.

4 Maso akunyada, ndi mtima wodzikuza, Ndi nyali ya oipa, ziri cimo.

5 Zoganizira za wakhama zicurukitsadi katundu; Koma yense wansontho angopeza umphawi.

6 Kupata cuma ndi lilime lonama ndiko nkhungu yoyendayenda, ngakhale misampha ya imfa.

7 Ciwawa ca amphulupulu cidzawakokolola; Cifukwa akana kucita ciweruzo.

8 Wosenza cimo njira yace ikhotakhota; Koma nchito ya woyera mtima ilungama.

9 Kukhala pa ngondya ya tsindwi kufunika Kuposa kukhala m'nyumba ndi mkazi wolongolola.

10 Wamphulupulu mtima wace umkhumba zoipa; Sakomera mtima mnzace.

11 Polangidwa wonyoza, wacibwana alandira nzeru, Naphunzira pakuyang'ana pa wanzeru.

12 Wolungama aganizira za nyumba ya wamphulupulu, Kuti amphulupulu amagwetsedwa, naona zoipa.

13 Wotseka makutu ace polira waumphawi, Nayenso adzalira koma osamvedwa.

14 Mphatso ya m'tseri ipembedza mkwiyo, Ndi mtulo wa pamfunga ukali wolimba.

15 Kucita ciweruzo kukondweretsa wolungama; Koma kuwaononga akucita mphulupulu,

16 Munthu wosocera pa njira ya nzeru Adzakhala m'msonkhano wa akufa.

17 Wokonda zoseketsa adzasauka; Wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.

18 Wocimwa ndiye ciombolo ca wolungama; Ndipo waciwembu adzalowa m'malo mwa oongoka mtima.

19 Kukhala m'cipululu kufunika Kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wong'ung'udza.

20 Mokhala wanzeru muli katundu wofunika ndi mafuta; Koma wopusa angozimeza.

21 Wolondola cilungamo ndi cifundo Apeza moyo, ndi cilungamo, ndi ulemu.

22 Wanzeru akwera pa mudzi wa olimba, Nagwetsa mphamvu yace imene anaikhulupirira.

23 Wosunga m'kamwa mwace ndi lilime lace Asunga moyo wace kumabvuto.

24 Wonyada wodzikuza dzina lace ndiye wonyoza; Acita mwaukali modzitama.

25 Cifuniro ca wolesi cimupha; Cifukwa manja ace akana kugwira nchito.

26 Ena asirira modukidwa tsiku lonse; Koma wolungama amapatsa osamana.

27 Nsembe ya oipa inyansa; Makamaka pakudza nayo iwo mwaciwembu.

28 Mboni yonama idzafa; Koma mwamuna wakumvetsa adzanena mosakayika,

29 Munthu woipa aumitsa nkhope yace; Koma woongoka mtima akonza njira zace.

30 Kulibe nzeru ngakhale luntha Ngakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.

31 Kavalo amakonzedweratu cifukwa ca tsiku la nkhondo; Koma wopulumutsa ndiye Yehova.

22

1 Mbiri yabwino ifunika kopambana cuma cambiri; Kukukomera mtima anzako kuposa siliva ndi golidi.

2 Wolemera ndi wosauka akumana, Wolenga onsewo ndiye Yehova.

3 Wocenjera aona zoipa, nabisala; Koma acibwana angopitirira, nalipitsidwa.

4 Mphotho ya cifatso ndi kuopa, Yehova Ndiye cuma, ndi ulemu, ndi moyo.

5 Minga ndi misampha iri m'njira ya wokhota; Koma wosunga moyo wace adzatarikira imeneyo.

6 Phunzitsa mwana poyamba njira yace; Ndipo angakhale atakalamba sadzacokamo.

7 Wolemera alamulira osauka; Ndipo wokongola ndiye kapolo wa womkongoletsa.

8 Wofesa zosalungama adzakolola tsoka; Ndipo ntyole ya mkwiyo wace idzalephera.

9 Mwini diso lamataya adzadala; Pakuti apatsa osauka zakudya zace.

10 Ukainga wonyoza, makangano adzaturuka; Makani ndi manyazi adzalekeka.

11 Wokonda kuyera mtima, Mfumu idzakhala bwenzi lace cifukwa ca cisomo ca milomo yace.

12 Maso a Yehova acinjiriza wodziwa; Koma agwetsa mau a munthu wa ziwembu.

13 Waulesi ati, Pali mkango panjapo, Ndidzaphedwa pamakwalalapo.

14 M'kamwa mwa mkazi waciwerewere muli dzenje lakuya; Yemwe Yehova amkwiyira adzagwamo.

15 Utsiru umangidwa mumtima mwa mwana; Koma ntyole yomlangira idzauingitsira kutari.

16 Wotsendereza waumphawi kuti acurukitse cuma cace, Ndi wopatsa wolemera kanthu, angosauka.

17 Chera makutu ako, numvere mau a anzeru, Nulozetse mtima wako kukadziwa zanga.

18 Pakuti mauwo akondweretsa ngati uwasunga m'kati mwako, Ngati akhazikika pamodzi pa milomo yako.

19 Ndakudziwitsa amenewo lero, ngakhale iwedi, Kuti ukhulupirire Yehova.

20 Kodi sindinakulembera zoposa Za uphungu ndi nzeru;

21 Kuti ukadziwitse ntheradi yace ya mau oona, Nukabwere ndi mau oona kwa iwo amene anakutumiza?

22 Usalande za waumphawi cifukwa ali waumphawi, Ngakhale kutsendereza wosauka kubwalo.

23 Pakuti Yehova adzanenera mlandu wao; Omwe akwatula zao Iye adzakwatula moyo wao.

24 Usayanjane ndi munthu wokwiya msanga; Ngakhale kupita ndi mwamuna waukali;

25 Kuti ungaphunzire mayendedwe ace, Ndi kutengera moyo wako msampha,

26 Usakhale wodulirana mpherere, Ngakhale kumperekera cikole ca ngongole zace.

27 Ngati ulibe cobwezera Kodi acotserenji kama lako pansi pako?

28 Usasunthe cidziwitso cakale ca m'malire, Cimene makolo ako anaciimika.

29 Kodi upenya munthu wofulumiza nchito zace? Adzaima pamaso pa mafumu, osaima pamaso pa anthu acabe.

23

1 Pamene ukhala ulinkudya ndi mkuru, Zikumbukira ameneyo ali pamaso pako;

2 Nuike mpeni pakhosi pako, Ngati uli wadyera.

3 Usakhumbe zolongosoka zace; Pokhala zakudya zonyenga.

4 Usadzitopetse kuti ulemere; Leka nzeru yako yako.

5 Kodi upenyeranji cimene kulibe? Pakuti cuma cunera mapiko, Ngati mphungu youluka mumlengalenga.

6 Usadye zakudya zace za wa maso ankhwenzule, Ngakhale kukhumba zolongosoka zace;

7 Pakuti monga asinkha m'kati mwace, ali wotere; Ati kwa iwe, Idya numwe; Koma mtima wace suli pa iwe.

8 Pakuti nthongo imene unaidya udzaisanza, Ndi kutaya mau ako okondweretsa.

9 Usalankhule m'makutu a wopusa; Pakuti adzapeputsa nzeru ya mau ako.

10 Usasunthe cidziwitso cakale ca m'malire; Ngakhale kulowa m'minda ya amasiye;

11 Pakuti Mombolo wao walimba; Adzawanenera mlandu wao pa iwe.

12 Lozetsa mtima wako kumwambo, Ndi makutu ako ku mau a nzeru.

13 Usamane mwana cilango; Pakuti ukammenya ndi ntyole safa ai.

14 Udzammenya ndi ntyole, Nudzapulumutsa moyo wace kunsi kwa manda.

15 Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru, Mtima wanga wa inedi udzakondwa;

16 Imso zanga zidzasangalala, Polankhula milomo yako zoongoka.

17 Mtima wako usacitire nsanje akucimwawo; Koma opabe Yehova tsiku lonse;

18 Pakutitu padzakhala mphotho; Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.

19 Tamvera tsopano, mwananga, utenge nzeru, Ulunjikitse mtima wako m'njiramo.

20 Usakhale mwa akumwaimwa vinyo, Ndi ankhuli osusuka.

21 Pakuti wakumwaimwa ndi wosusukayo adzasauka; Ndipo kusinza kudzabveka munthu nsanza.

22 Tamvera atate wako anakubala, Usapeputse amako atakalamba.

23 Gula ntheradi, osaigulitsa; Nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.

24 Atate wa wolungama adzasekeradi; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.

25 Atate wako ndi amako akondwere, Amako wakukubala asekere.

26 Mwananga, undipatse mtima wako, Maso ako akondwere ndi njira zanga,

27 Pakuti mkazi wadama ndiye dzenje lakuya; Ndipo mkazi waciwerewere ndiye mbuna yopapatiza.

28 Pakuti abisalira ngati wacifwamba, Nacurukitsa anthu a ciwembu.

29 Ndani ali ndi cisoni? ndani asauka? ndani ali ndi makangano? Ndani ang'ung'udza? ndani alasidwa cabe? ndani afiira maso?

30 Ngamene acedwa pali vinyo, Napita kukafunafuna vinyo wosanganizidwa.

31 Usayang'ane pavinyo alikufiira. Alikung'azimira m'cikho. Namweka mosalala.

32 Pa citsiriziro cace aluma ngati njoka, Najompha ngati mamba.

33 Maso ako adzaona zacilendo, Mtima wako udzalankhula zokhota.

34 Udzafanana ndi wina wogona pakati pa nyanja, Pena wogona pa nsonga ya mlongoti wa ngalawa.

35 Udzati, Anandimenya, osaphwetekedwa ine; Anandikwapula, osamva ine; Ndidzauka nthawi yanji? Ndidzafuna-funanso vinyoyo.

24

1 Usacitire nsanje anthu oipa, Ngakhale kufuna kukhala nao;

2 Pakuti mtima wao ulingalira za cionongeko; Milomo yao ilankhula za mphulupulu.

3 Nzeru imangitsa nyumba; Luntha liikhazikitsa.

4 Kudziwa kudzaza zipinda zace Ndi cuma conse cofunika ca mtengo wace.

5 Mwamuna wanzeru ngwamphamvu; Munthu wodziwa ankabe nalimba.

6 Pakuti udzaponya nkhondo yako ndi upo, Ndi kupulumuka pocuruka aphungu,

7 Nzeru itarikira citsiru; Satsegula pakamwa kubwalo.

8 Wolingalira zakucita zoipa Anthu adzamcha waciwembu.

9 Maganizo opusa ndiwo cimo; Wonyoza anyansa anthu.

10 Ukalefuka tsiku la tsoka Mphamvu yako icepa.

11 Omwe atengedwa kuti akafe, uwapulumutse; Omwe ati aphedwe, usaleke kuwalanditsa.

12 Ukanena, Taonani, sitinadziwa cimeneci; Kodi woyesa mitima sacizindikira ici? Ndi wosunga moyo wako kodi sacidziwa? Ndipo kodi sabwezera munthu yense monga mwa macitidwe ace?

13 Mwananga, idya uci pakuti ngwabwino, Ndi cisa cace citsekemera m'kamwamwako;

14 Potero udzadziwa kuti nzeru iri yotero m'moyo wako; Ngati waipeza padzakhala mphotho, Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.

15 Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama; Usapasule popuma iyepo.

16 Pakuti wolungama amagwa kasanu ndi kawiri, nanyamukanso; Koma oipa akhumudwa pomfikira tsoka.

17 Usakondwere pakugwa mdani wako; Mtima wako usasekere pokhumudwa iye;

18 Kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa, Ndi kuleka kumkwiyira.

19 Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa; Ngakhale kucitira nsanje amphulupulu;

20 Pakuti woipayo sadzalandira mphotho; Nyali ya amphulupulu idzazima.

21 Mwananga, opa Yehova ndi mfumu yomwe, Osadudukira anthu osinthasintha.

22 Pakuti tsoka lao lidzaoneka modzidzimuka; Ndipo ndani adziwa cionongeko ca zaka zao?

23 Izinso ziri za anzeru. Poweruza cetera siliri labwino.

24 Wonenakwa woipa, Wolungama iwe; Magulu a anthu adzamtemberera, mitundu ya anthu idzamkwiyira,

25 Omwe amdzudzula adzasekera, Nadzadalitsika ndithu.

26 Wobwezera mau oongoka Apsompsona milomo.

27 Longosola nchito yako panjapo, nuikonzeretu kumunda; Pambuyo pace ndi kumanga nyumba yako.

28 Usacitire mnzako umboni womtsutsa opanda cifukwa; Kodi udzanyenga ndi milomo yako?

29 Usanene, Ndidzamcitira zomwezo anandicitira ine; Ndidzabwereza munthuyo monga mwa macitidwe ace.

30 Ndinapita pa munda wa wolesi, Polima mphesa munthu wosowa nzeru.

31 Taonani, ponsepo panamera minga, Ndi kuwirirapo khwisa; Chinga lace lamiyala ndi kupasuka.

32 Pamenepo ndinayang'ana ndi kuganizira, Ndinaona ndi kulandira mwambo.

33 Tulo tapang'ono, kungoodzera pang'ono, Kungomanga manja pang'ono m'kugona,

34 Ndipo umphawi wako udzafika ngati mbala; Ndi kusauka kwako ngati munthu wacikopa.

25

1 Iyinso ndiyo miyambo ya Solomo Imene anthu a Hezekiya mfumu ya Yuda anailemba.

2 Kubisa kanthu ndi ulemerero wa Mulungu; Koma ulemerero wa mafumu ndi kusanthula kanthu.

3 Pamlengalenga patarika, ndi padziko pakuya, Koma mitima ya mafumu singasanthulike.

4 Cotsera siliva mphala yace, Mmisiri wa ng'anjo aturutsamo mbale;

5 Cotsera woipa pamaso pa mfumu, Mpando wace udzakhazikika m'cilungamo.

6 Usadzitame pamaso pa mfumu, Ngakhale kuima m'malo mwa akuru;

7 Pakuti kunena kwa iwe, Takwera kuno, Kupambana ndi kuti utsitsidwe pamaso pa kalonga, Amene maso ako anamuona.

8 Usaturuke mwansontho kukalimbana, Ungalephere pa kutha kwace, Atakucititsa mnzako manyazi.

9 Nena mlandu wako ndi mnzako, Osaulula zinsinsi za mwini;

10 Kuti wakumva angakutonze, Mbiri yako yoipa ndi kusacoka.

11 Mau oyenera a pa nthawi yace Akunga zipatso zagolidi m'nsengwa zasiliva.

12 Monga phelele lagolidi ndi cipini cagolidi woyengeka, Momwemo wanzeru wodzudzula pa khutu lomvera.

13 Monga cisanu ca cipale cofewa pa nthawi ya masika, Momwemo mthenga wokhulupirika kwa amene anamtuma; Atsitsimutsa moyo wa ambuyace.

14 Monga mitambo ndi mphepo popanda mvula, Momwemo ndiye wodzikweza ndi zipatso zace monyenga.

15 Cipiriro cipembedza mkuru; Lilime lofatsa lityola pfupa,

16 Wapeza uci kodi? Idyapo wokwanira, Kuti ungakukole, nusanze.

17 Phazi lako lilowe m'nyumba ya mnzako kamodzi kamodzi; Kuti angatope nawe ndi kukuda.

18 Wocitira mnzace umboni wonama Ndiye cibonga, ndi lupanga, ndi mubvi wakuthwa.

19 Kukhulupirira munthu wa ciwembu tsiku latsoka Kunga dzino lotyoka ndi phazi loguluka.

20 Monga wobvula maraya tsiku lamphepo, Ngakhale kuthira vinyo wosasa m'soda, Momwemo woyimbira nyimbo munthu wacisoni.

21 Mdani wako akamva njala umdyetse, Akamva ludzu ummwetse madzi,

22 Pakuti udzaunjika makala amoto pamtu pace; Ndipo Yehova adzakupatsa mphotho,

23 Mphepo ya kumpoto ifikitsa mvula; Comweco lilime losinjirira likwiyitsa nkhope.

24 Kukhala pa ngondya ya tsindwi kufunika Kuposa kukhala m'nyumba ndi mkazi wolongolola.

25 Monga madzi ozizira kwa munthu wotopa, Momwemo mau abwino akucokera ku dziko lakutari.

26 Monga kasupe wopondedwa, ndi citsime cobvonongeka, Momwemo wolungama ngati akonjera woipa.

27 Kudya uci wambiri sikuli kwabwino; Comweco kufunafuna ulemu wako wako sikuli ulemu.

28 Wosalamulira mtima wace Akunga mudzi wopasuka wopanda linga,

26

1 Monga cipale cofewa m'malimwe, ndi mvula m'masika, Momwemo ulemu suyenera citsiru.

2 Monga mpheta irikuzungulira, ndi namzeze alikuuluka, Momwemo temberero la pacabe silifikira.

3 Cikoti ciyenera kavalo, ndi cam'kamwa ciyenera buru, Ndi ntyole iyenera pamsana pa zitsiru.

4 Usayankhe citsiru monga mwa utsiru wace, Kuti ungafanane naco iwe wekha.

5 Yankha citsiru monga mwa utsiru wace, Kuti asadziyese wanzeru.

6 Wotumiza mau ndi dzanja la citsiru Adula mapazi ace, namwa zompweteka.

7 Miyendo ya wopunduka iri yolobodoka, Momwemo mwambi m'kamwa mwa zitsiru.

8 Monga thumba la ngale m'mulu wa miyala, Momwemo wocitira citsiru ulemu.

9 Monga munga wolasa dzanja la woledzera, Momwemo mwambi m'kamwa mwa zitsiru.

10 Monga woponya mibvi ndi kulasa onse, Momwemo wolembera citsiru, ndi wolembera omwe alikupita panjira.

11 Monga garu abweranso ku masanzi ace, Momwemo citsiru cicitanso zopusa zace.

12 Kodi uona munthu wodziyesa wanzeru? Ngakhale citsiru cidzacenjera koma ameneyo ai.

13 Wolesi ati, Mkango uli panjira, Wobangulawo uli m'makwalala.

14 Monga citseko cikankhikira pa zitsulo za pamphuthu, Momwemo wolesi agubuduka pakama pace.

15 Wolesi alonga dzanja lace m'mbale; Kumtopetsa kulibweza kukamwa kwace.

16 Wolesi adziyesa wanzeru Koposa anthu asanu ndi awiri akuyankha mozindikira.

17 Wakungopita ndi kubvutika ndi ndeu yosakhala yace Akunga wogwira makutu a garu.

18 Monga woyaruka woponya nsakali, Mibvi, ndi imfa,

19 Momwemo wonyenga mnzace ndi kuti, Ndi kusewera kumeneku.

20 Posowa nkhuni moto ungozima; Ndi popanda kazitape makangano angoleka.

21 Monga makala ozizira pa makala akunyeka, ndi nkhuni pamoto; Momwemo munthu wamakangano autsa ndeu.

22 Mau a kazitape ndi zakudya zolongosoka Zitsikira m'kati mwa mimba.

23 Milomo yofunitsitsa ndi mtima woipa Ikunga mbale yadothi anaimata ndi mphala yasiliva.

24 Wakuda mnzace amanyenga ndi milomo yace; Koma akundika cinyengo m'kati mwace;

25 Pamene akometsa mau ace usamkhulupirire; Pakuti m'mtima mwace muli zonyansa zisanu ndi ziwiri.

26 Angakhale abisa udani wace pocenjera, Koma udio wace udzabvumbulutsidwa posonkhana anthu.

27 Wokumba dzenje adzagwamo, Wogubuduza mwala, udzabweranso pa iye mwini.

28 Lilime lonama lida omwewo linawasautsa; Ndipo m'kamwa mosyasyalika mungoononga.

27

1 Usanyadire zamawa, Popeza sudziwa tsiku lina lidzabala ciani?

2 Wina akutame, si m'kamwamwako ai; Mlendo, si milomo ya iwe wekha.

3 Mwala ulemera, mcenga ndiwo katundu; Koma mkwiyo wa citsiru upambana kulemera kwace.

4 Kupweteka mtima nkwa nkhanza, mkwiyo usefuka; Koma ndani angalakike ndi nsanje?

5 Cidzudzulo comveka ciposa cikondi cobisika.

6 Kulasa kwa bwenzi kulikokhulupirika; Koma mdani apsompsona kawiri kawiri.

7 Mtima wokhuta upondereza cisa ca uci; Koma wakumva njala ayesa zowawa zonse zotsekemera.

8 Monga mbalame yosocera ku cisa cace, Momwemo munthu wosocera ku malo ace.

9 Mafuta ndi zonunkhira zikondweretsa mtima, Ndi ubwino wa bwenzi uteronso pakupangira uphungu,

10 Mnzako, ndi mnzace wa atate wako, usawasiye; Usanke ku nyumba ya mbale wako tsiku la tsoka lako; Mnansi wapafupi aposa mbale wakutari.

11 Mwananga, khala wanzeru, nukondweretse mtima wanga; Kuti ndimuyankhe yemwe anditonza.

12 Wocenjera aona zoipa, nabisala; Koma acibwana angopitirira, nalipitsidwa.

13 Tenga maraya a woperekera mlendo cikole; Woperekera mkazi waciwerewere cikole umgwire mwini.

14 Yemwe adalitsa mnzace ndi mau akuru pouka mamawa, Anthu adzaciyesa cimeneco temberero.

15 Kudonthadontha tsiku lamvula, Ndi mkazi wolongolola ali amodzimodzi.

16 Wofuna kumletsayo afuna kuletsa mphepo; Dzanja lace lamanja lingogwira mafuta.

17 Citsulo cinola citsulo; Comweco munthu anola nkhope ya mnzace.

18 Wosunga mkuyu adzadya zipatso zace; Wosamalira ambuyace adzalemekezedwa.

19 Monga m'madzi nkhope zionana, Momwemo mitima ya anthu idziwana.

20 Kunsi kwa manda ndi kucionongeko sikukhuta; Ngakhale maso a munthu sakhutai.

21 Siliva asungunuka m'mbiya, Ndi golidi m'ng'anjo, Motero comwe munthu acitama adziwika naco.

22 Ungakhaleukonolacitsirum'mtondo ndi munsi, pamodzi ndi mphale, Koma utsiru wace sudzamcoka.

23 Udziwitsitse zoweta zako ziri bwanji, Samalira magulu ako;

24 Pakuti cuma siciri cosatha; Kodi korona alipobe mpaka mibadwo mibadwo?

25 Amatuta maudzu, msipu uoneka, Achera masamba a kumapiri,

26 Ana a nkhosa akubveka, Atonde aombolera munda;

27 Mkaka wa mbuzi udzakukwanira kudya; Ndi a pa banja lako ndi adzakazi ako.

28

1 Woipaathawapalibewomthamangitsa; Koma olungama alimba mtima ngati mkango.

2 Pocimwa dziko akalonga ace acuruka; Koma anthu ozindikira ndi odziwa alikhazikikitsa nthawi yaikuru.

3 Munthu waumphawi wotsendereza osauka Akunga mvula yamadzi yokokolola dzinthu.

4 Omwe asiya cilamulo atama oipa; Koma omwe asunga cilamulo akangana nao.

5 Oipa samvetsetsa ciweruzo; Koma omwe afuna Yehova amvetsetsa zonse.

6 Waumphawi woyenda mwangwiro Apambana ndi yemwe akhotetsa njira zace, angakhale alemera.

7 Wosunga cilamulo ndiye mwana wozindikira; Koma mnzao wa adyera acititsa atate wace manyazi.

8 Wocurukitsa cuma cace, pokongoletsa ndi phindu, Angokundikira yemwe acitira osauka cisoni.

9 Wopewetsa khutu lace kuti asamve cilamulo, Ngakhale pemphero lace linyansa.

10 Wosoceretsa oongoka mtima alowe m'njira yoipa, Adzagwa mwini m'dzenje lace; Koma angwiro adzalandira colowa cabwino.

11 Wolemera adziyesa wanzeru; Koma wosauka wozindikira aululitsa zace.

12 Posekera olungama pali ulemerero wambiri; Koma pouka oipa anthu amabisala.

13 Wobisa macimo ace sadzaona mwai; Koma wakuwabvomereza, nawasiya adzacitidwa cifundo.

14 Wodala munthu wakuopakosalekeza; Koma woumitsa mtima wace adzagwa m'zoipa.

15 Monga mkango wobangula ndi cirombo coyendayenda, Momwemo mfumu yoipa ya anthu osauka.

16 Kalonga wosowa nzeru apambana kusautsa; Koma yemwe ada cisiriro adzatanimphitsa moyo wace.

17 Woparamula mlandu wakupha munthu adzathawira kudzenje; Asamuletse.

18 Woyenda mwangwiro adzapulumuka; Koma wokhota m'mayendedwe ace adzagwa posacedwa.

19 Wolima munda wace zakudya zidzamkwanira; Koma wotsata anthu opanda pace umphawi udzamkwanira.

20 Munthu wokhulupirika ali ndi madalitso ambiri; Koma wokangaza kulemera sadzapulumuka cilango,

21 Cetera siliri labwino, Ngakhale kulakwa kuti ukadye kanthu.

22 Mwini diso lankhwenzule akangaza kulemera, Osadziwa kuti umphawi udzamfikira.

23 Adzamkomera mtima wodzudzula m'tsogolo mwace, Koposa wosyasyalika ndi lilime lace.

24 Wobera atate wace, pena amace, nati, Palibe kulakwa; Ndiye mnzace wa munthu wopasula.

25 Wodukidwa mtima aputa makangano; Koma wokhulupirira Yehova adzakula.

26 Wokhulupirira mtima wace wace ali wopusa; Koma woyenda mwanzeru adzapulumuka,

27 Wogawira aumphawi sadzasowa; Koma wophimba maso ace adzatembereredwa kwambiri.

28 Pouka oipa anthu amabisala; Koma pakufa amenewo olungama acuruka.

29

1 Yemwe aumitsa khosi atadzudzulidwa kwambiri, Adzasweka modzidzimuka, palibe comciritsa.

2 Pocuruka olungama anthu akondwa; Koma polamulira woipa anthu ausa moyo.

3 Mwamuna wokonda nzeru akondweretsa atate wace; Koma wotsagana ndi akazi adama amwaza cuma.

4 Mfumu akhazikitsa dziko ndi ciweruzo; Koma wosonkhetsa anthu mphatso alipululutsa.

5 Wosyasyalika mnzace Acherera mapazi ace ukonde.

6 M'kulakwa kwa woipa muli msampha; Koma wolungama ayimba, nakondwera.

7 Wolungama asamalira mlandu wa osauka; Koma woipa alibe nzeru yakuudziwa.

8 Anthu onyoza atentha mudzi; Koma anzeru alezetsa mkwiyo.

9 Munthu wanzeru akatsutsana ndi munthu wopusa, Ngakhale akwiya, ngakhale aseka, palibe mtendere.

10 Anthu ankhanza ada wangwiro; Koma oongoka mtima asamalira moyowace.

11 Citsiru cibvumbulutsa mkwiyo wace wonse; Koma wanzeru auletsa nautontholetsa.

12 Mkuru akamvera cinyengo, Atumuki ace onse ali oipa,

13 Waumphawi ndi wotsendereza akumana; Yehova apenyetsa maso a onse awiriwo.

14 Mfumu yolamulira osauka mwantheradi, Mpando wace udzakhazikika kufikira nthawi zonse.

15 Ntyole ndi cidzudzulo zipatsa nzeru; Koma mwana womlekerera acititsa amace manyazi.

16 Pocuruka oipa zolakwa zicuruka; Koma olungama adzaona kugwa kwao.

17 Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa; Nadzasangalatsa moyo wako.

18 Popanda cibvumbulutso anthu amasauka; Koma wosunga cilamulo adalitsika.

19 Kapolo sangalangizidwe ndi mau, Pakuti azindikira koma osabvomera.

20 Kodi uona munthu wansontho m'mau ace? Ngakhale citsiru cidzacenjera, koma ameneyo ai.

21 Yemwe alera kapolo wace mwa ufulu kuyambira ubwana wace, Pambuyo pace adzadziyesa mwana wobala.

22 Mwamuna wamkwiyo aputa makangano; Waukali acuruka zolakwa.

23 Kudzikuza kwa munthu kudzamcepetsa; Koma wokhala ndi mtima wodzicepetsa adzalemekezedwa.

24 Woyenda ndi mbala ada moyo wace wace; Amva kulumbira, koma osaulula kanthu.

25 Kuopa anthu kuchera msampha; Koma wokhulupirira Yehova adzapulumuka,

26 Ambiri afunafuna ciyanjano ca mkuru; Koma ciweruzo ca munthu cicokera kwa Yehova.

27 Munthu woipa anyansa olungama; Ndipo woongoka m'njira anyansa wocimwa.

30

1 Mau a Aguri mwana wa Yake; uthenga. Munthuyo anati, Ndadzitopetsa, Mulungu; Ndadzitopetsa, Mulungu, ndathedwa;

2 Pakuti ndipambana anthu onse kupulukira, Ndiribe luntha la munthu.

3 Sindinaphunzira nzeru Ngakhale kudziwa Woyerayo.

4 Ndani anakwera kumwamba natsikanso? Ndani wakundika nafumbata mphepo? Ndani wamanga madzi m'maraya ace? Ndani wakhazikitsa matsiriziro onse a dziko? Dzina lace ndani? dzina la mwanace ndani? kapena udziwa.

5 Mau onse a Mulungu ali oyengeka; Ndiye cikopa ca iwo amene amkhulupirira.

6 Usaoniezere kanthu pa mau ace, Angakudzudzule, nungatsutsidwe kuti ulikunama.

7 Zinthu ziwiri ndakupemphani, Musandimane izo ndisanamwalire:

8 Mundicotsere kutari zacabe ndi mabodza; Musandipatse umphawi, ngakhale cuma, Mundidyetse zakudya zondiyenera;

9 Ndingakhute ndi kukukanani, ndi kuti, Yehova ndani? Kapena ndingasauke ndi kuba, Ndi kuchula dzina la Mulungu wanga pacabe.

10 Usanamizire kapolo kwa mbuyace, Kuti angakutemberere nawe ndi kutsutsidwa.

11 Pali mbadwo wotemberera atate ao, Osadalitsa amao.

12 Pali mbadwo wodziyesa oyera, Koma osasamba litsilo lao.

13 Pali mbadwo wokwezatu maso ao, Zikope zao ndi kutukula.

14 Pali mbadwo mano ao akunga malupanga, zibwano zao zikunga mipeni; Kuti adye osauka kuwacotsa kudziko, ndi aumphawi kuwacotsa mwa anthu.

15 Msundu uli ndi ana akazi awiri ati, Patsa, patsa, Pali zinthu zitatu sizikhuta konse, Ngakhale zinai sizinena, Kwatha:

16 Manda, ndi cumba, Dziko losakhuta madzi, Ndi moto wosanena, Kwatha.

17 Diso locitira atate wace ciphwete, ndi kunyoza kumvera amace, Makungubwi a kumtsinje adzalikolowola, ana a mphungu adzalidya,

18 Zinthu zitatu zindithetsa nzeru, Ngakhale zinai, sindizidziwa:

19 Njira ya mphungu m'mlengalenga, Njira ya njoka pamwala, Njira ya ngalawa pakati pa nyanja. Njira ya mwamuna ndi namwali.

20 Comweco njira ya mkazi wacigololo; Adya, napukuta pakamwa, nati, Sindinacita zoipa,

21 Cifukwa ca zinthu zitatu dziko linthunthumira; Ngakhale cifukwa ca zinai silingathe kupirira nazo:

22 Cifukwa ca kapolo pamene ali mfumu; Ndi citsiru citakhuta zakudya;

23 Cifukwa ca mkazi wodedwa wokwatidwa; Ndi mdzakazi amene adzalandira colowa ca mbuyace.

24 Ziripo zinai ziri zazing'ono padziko; Koma zipambana kukhala zanzeru:

25 Nyerere ndi mtundu wosalimba, Koma zitengeratu zakudya zao m'malimwe.

26 Mbira ndi mtundu wopanda mphamvu, Koma ziika nyumba zao m'matanthwe.

27 Dzombe liribe mfumu, Koma lituruka lonse mabwalo mabwalo.

28 Buluzi ungamgwire m'manja, Koma ali m'nyumba za mafumu.

29 Pali zinthu zitatu ziyenda cinya cinya; Ngakhale zinai ziyenda mwaufulu:

30 Mkango umene uposa zirombo kulimba, Supambukira cinthu ciri conse;

31 Kavalo wolimba m'cuuno, ndi tonde, Ndi mfumu yokhala ndi ankhondo ace.

32 Ngati wapusa podzikweza, Ngakhale kuganizira zoipa, tagwira pakamwa.

33 Pakuti potakasa mkaka, mafuta ayengekapo; Ndi popsinja mpfuno, mwazi uturukamo; Ndi potimbikira mkwiyo ndeu ionekamo.

31

1 Mau a Lemueli mfumu, uthenga umene amace anamphunzitsa.

2 Ciani mwananga, Ciani mwana wa mimba yanga? Ciani mwana wa zowinda zanga?

3 Musapereke mphamvu yako kwa akazi, Ngakhale kuyenda m'njira yoononga mafumu.

4 Mafumu, Lemueli, mafumu sayenera kumwa vinyo; Akalonga sayenera kunena, Cakumwa caukali ciri kuti?

5 Kuti angamwe, naiwale malamulo, Naweruze mokhota anthu onse osautsidwa.

6 Wofuna kufa umpatse cakumwa caukali, Ndi vinyo kwa owawa mtima;

7 Amwe, narwale umphawi wace, Osakumbukiranso bvuto lace.

8 Tsegula pakamwa pako, ukanenere wosalankhula, Ndi mlandu wa amasiye onse.

9 Tsegula pakamwa pako, Nuweruze molungama, nunenere osauka ndi aumphawi.

10 Mkazi wangwiro ndani angampeze? Pakuti mtengo wace uposa ngale.

11 Mtima wa mwamuna wace umkhulupirira, Sadzasowa phindu.

12 Mkaziyo amcitira zabwino, si zoipa, Masiku onse a moyo wace.

13 Afuna ubweya ndi thonje, Nacita mofunitsa ndi manja ace.

14 Akunga zombo za malonda; Nakatenga zakudya zace kutari.

15 Aukanso kusanace, Napatsa banja lace zakudya, nagawira adzakazi ace nchito.

16 Asinkhasinkha za munda, naugula; Naoka mipesa ndi zipatso za manja ace.

17 Amanga m'cuuno mwace ndi mphamvu, Nalimbitsa mikono yace,

18 Azindikira kuti malonda ace ampindulira; Nyali yace sizima usiku.

19 Agwira njinga ya thonje ndi dzanja lace, Nafumbata mtengo wace.

20 Aolowera cikhato cace osauka; Natambasulira aumphawi manja ace.

21 Saopera banja lace cipale cofewa; Pakuti banja lace lonse libvala mlangali.

22 Adzipangira zimbwi zamaangamaanga; Nabvala bafuta ndi guta woti biriwiri.

23 Mwamuna wace adziwika kubwalo, Pokhala pakati pa akuru a dziko.

24 Asoka maraya abafuta, nawagulitsa; Napereka mipango kwa wogulitsa malonda.

25 Abvala mphamvu ndi ulemu; Nangoseka nthawi ya m'tsogolo.

26 Atsegula pakamwa pace ndi nzeru, Ndipo cilangizo ca cifundo ciri pa lilime lace.

27 Ayang'anira mayendedwe a banja lace, Sadya zakudya za ulesi.

28 Anace adzanyamuka, nadzamucha wodala; Mwamuna wace namtama, nati,

29 Ana akazi ambiri anacita mwangwiro, Koma iwe uposa onsewo.

30 Kukongola kungonyenga, maonekedwe okoma ndi cabe; Koma mkazi woopa Yehova adzatamandidwa.

31 Mumpatse zipatso za manja ace; Ndi nchito zace zimtame kubwalo.