1

1 TAONANI Teofilo inu, mau aja oyamba ndinakonza, za zonse Yesu anayamba kuzicita ndi kuziphunzitsa,

2 kufikira tsiku lija anatengedwa kunka Kumwamba, atatha kulamulira mwa Mzimu Woyera atumwi amene adawasankha;

3 kwa iwonso anadzionetsera yekha wamoyo ndi zitsimikizo zambiri, zitatha zowawa zace, naonekera kwa iwo masiku makumi anai, ndi kunena zinthu za Ufumuwa Mulungu;

4 ndipo e posonkhana nao pamodzi, anawalamulira asacoke ku Yerusalemu, komatu alindire lonjezano la Atate, limene, anati, munalimva kwa Ine;

5 pakuti Yohane anabatizadi ndi madzi; koma inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera, asanapite masiku ambiri.

6 Pamenepo iwowa, atasonkhana pamodzi, anamfunsa iye, nanena, Ambuye, kodi nthawi yino mubwezera ufumu kwa Israyeli?

7 Koma anati kwa iwo, Sikuli kwa inu kudziwa nthawi kapena nyengo, zimene Atate anaziika m'ulamuliro wace wa iye yekha.

8 Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo mudzakhala mboni zanga m'Yerusalemu, ndi m'Yudeya lonse, ndi m'Samariya, ndi kufikira malekezero ace a dziko.

9 Ndipo m'mene adanena izi, ali cipenyerere iwo, ananyamulidwa; ndipo mtambo unamlandira iye kumcotsa kumaso kwao.

10 Ndipo pakukhala iwo cipenyerere kumwamba pomuka iye, taonani, amuna awiri obvala zoyera anaimirira pambali pao;

11 amenenso anati, Amuna a ku Galileya, muimiranji ndi kuyang'ana kumwamba? Yesu amene walandiridwa kunka Kumwamba kucokera kwa inu, adzadza momwemo monga munamuona alinkupita Kumwamba.

12 Pamenepo anabwera ku Yerusalemu kucokera ku phiri lonenedwa la Azitona, limene liyandikana ndi Yerusalemu, loyendako tsiku la Sabata.

13 Ndipo pamene adalowa, anakwera ku cipinda ca pamwamba, kumene analikukhalako; ndiwo Petro ndi Yohane ndi Yakobo ndi Andreya, Filipo ndi Tomasi, Bartolomeyu ndi Mateyu, Yakobo mwana wa Alifeyu, ndi Simoni Zelote, ndi Yuda mwana wa Yakobo.

14 Iwo onse analikukangalika m'kupemphera, pamodzi ndi akazi, ndi Mariya, amace wa Yesu, ndi abale ace omwe.

15 Ndipo m'masiku awa anaimirira Petro pakati pa abale, nati (gulu la anthu losonkhana pamalo pomwe ndilo ngati zana limodzi ndi makumi awiri),

16 Amuna inu, abale, kunayenera kuti lemba likwanitsidwe, limene Mzimu Woyera anayamba kunena mwa m'kamwa mwa Davine za Yudase, wokhala mtsogoleri wa iwo adagwira Yesu.

17 Cifukwa anali wowerengedwa mwa ife, ndipo analandira gawo lace la utumiki uwu.

18 (Uyutu tsono anadzitengera kadziko ndi mphoto ya cosalungama; ndipo anagwa camutu, naphulika pakati, ndi matumbo ace onse anakhuthuka;

19 ndipo cinadziwika ndi onse akukhala ku Yerusalemu; kotero kuti m'manenedwe ao kadzikoka kanachedwa Akeldama, ndiko, kadziko ka mwazi.)

20 Pakuti kwalembedwa m'buku la Masalmo, Pogonera pace pakhale bwinja, Ndipo pasakhale munthu wogonapo; Ndipo uyang'aniro wace autenge wina.

21 Potero kuyenera kuti wina wa amunawo anatsatana nafe nthawi yonseyi Ambuye Yesu analowa naturuka mwa ife,

22 kuyambira ubatizo wa Yohane, kufikira tsiku lija anatengedwa kunka Kumwamba kutisiya ife, mmodzi wa awa akhale mboni ya kuuka kwace pamodzi ndi ife.

23 Ndipo anaimikapo awiri, Yosefe wochedwa Barsaba, amene anachedwanso Yusto, ndi Matiya.

24 Ndipo anapemphera, nati, Inu, Ambuye, wozindikiramitima ya onse, sonyezani mwa awa awiri mmodziyo amene munamsankha,

25 alowe malo a utumiki uwu ndi utumwi, kucokera komwe Yudase anapatukira, kuti apite ku malo a iye yekha.

26 Ndipo anayesa maere pa iwo; ndipo anagwera Matiya; ndipo anawerengedwa pamodzi ndi khumi ndi mmodziwo.

2

1 Ndipo pakufika tsiku la Penteskoste, anali onse pamodzi pa malo amodzi.

2 Ndipo mwadzidzidzi anamveka mau ocokera Kumwamba ngati mkokomo wa mphepo yolimba, nadzaza nyumba yonse imene analikukhalamo.

3 Ndipo anaonekera kwa iwo malilime ogawanikana, onga amoto; ndipo unakhala pa iwo onse wayekha wayekha.

4 Ndipo anadzazidwa onse ndi Mzimu Woyera, nayamba kulankhula ndi malilime ena, monga Mzimu anawalankhulitsa.

5 Koma anali m'Yerusalemu okhalako Ayuda, amuna opembedza, ocokera ku mtundu uli wonse pansi pa thambo.

6 Koma pocitika mau awa, unyinji wa anthu unasonkhana, nusokonezedwa, popeza yense anawamva alikulankhula m'cilankhulidwe cace ca iye yekha.

7 Ndipo anadabwa onse, nazizwa, nanena, Taonani, awa onse alankhulawa sali Agalileya kodi?

8 ndipo nanga ife timva bwanji, yense m'cilankhulidwe cathu cimene tinabadwa naco?

9 Aparti ndi Amedi, ndi Aelami, ndi iwo akukhala m'Mesopotamiya, m'Yudeya, ndiponso m'Kapadokiya, m'Ponto, ndi m'Asiya;

10 m'Frugiya, ndiponso m'Pamfuliya, m'Aigupto, ndi mbali za Libiya wa ku Kurene, ndi alendo ocokera ku Roma, ndiwo Ayuda, ndiponso opinduka,

11 Akrete, ndi Aarabu, tiwamva iwo alikulankhula m'malilime athu zazikuru za Mulungu.

12 Ndipo anadabwa onse, nathedwa nzeru, nanena wina ndi mnzace, Kodi ici nciani?

13 koma ena anawaseka, nanena kuti, Akhuta vinyo walero.

14 Koma Petro, anaimirira pamodzi ndi khumi ndi mmodziwo, nakweza mau ace, nanena kwa iwo, nati, Amuna inu Ayuda, ndi inu nonse akukhala kwanu m'Yerusalemu, ici cizindikirike kwa inu, ndi po cherani khutu mau anga.

15 Pakuti awa sanaledzera monga muyesa inu; pakuti ndi ora lacitatulokha la tsiku;

16 komatu ici ndi cimene cinanenedwa ndi mneneri Yoeli,

17 Ndipo kudzali m'masiku otsiriza, anena Mulungu, Ndidzathira ca Mzimu wansa pa thupi liri lonse, Ndipo ana anu amuna, ndi akazi adzanenera, Ndipo anyamata anu adzaona masomphenya, Ndi akulu anu adzalota maloto;

18 Ndiponso pa akapolo anga ndi pa adzakazi anga m'masiku awa Ndidzathira ca Mzimu wanga; ndipo adzanenera.

19 Ndipo ndidzapatsa zodabwitsa m'thambo la kumwamba, Ndi zizindikilo pa dziko lapansi; Mwazi, ndi moto, ndi mpweya wautsi;

20 Dzuwa lidzasanduka mdima, Ndi mweziudzasanduka mwazi, Lisanadze tsiku la Ambuye, Lalikuru ndi loonekera;

21 Ndipo kudzali, kuti yense amene akaitana pa dzina la Ambuye adzapulumutsidwa.

22 Amuna inu Aisrayeli, mverani mau awa: Yesu Mnazarayo, mwamuna wocokera kwa Mulungu, wosonyezedwa kwa inu ndizimphamvu, ndi zozizwa, ndi zizindikilo, zimene Mulungu anazicita mwa iye pakati pa inu, monga mudziwa nokha;

23 ameneyo, woperekedwa ndi uphungu woikidwa ndi kudziwiratu kwa Mulungu, inu mwampacika ndi kumupha ndi manja a anthu osayeruzika;

24 yemweyo Mulungu anamuukitsa, atamasula zowawa za imfa, mwakuti sikunali kotheka kuti iye agwidwe nayo.

25 Pakuti Davine anena za Iye, Ndinaona Mbuye pamaso panga nthawi zonse; Cifukwa ali pa dzanja langa lamanja, kuti ndingasinthike;

26 Mwa ici unakondwera mtima wanga, ndipo linasangalala lilime langa; Ndipo thupi langanso lidzakhala m'ciyembekezo.

27 Pakuti simudzasiya moyo wanga ku Hade, Kapena simudzapereka Woyera wanu aone cibvunde,

28 Munandidziwitsa ine njira za moyo; Mudzandidzaza ndi kukondwera pamaso panu.

29 Amuna inu, abale, kuloleka kunena poyera posaopa kwa inu za kholo lija Davine, kuti adamwalira naikidwanso, ndipo manda ace ali ndi ife kufikira lero lino.

30 Potero, pokhala mneneri iye, ndi kudziwa kuti ndi Iumbiro anamlumbirira Mulungu, kuti mwa cipatso ca m'cuuno mwace adzakhazika wina pa mpando wacifumu wace;

31 iye pakuona ici kale, analankhula za kuuka kwa Kristu, kuti sanasiyidwa m'Hade, ndipo thupi lace silinaona cibvunde.

32 Yesu ameneyo, Mulungu anamuukitsa; za ici tiri mboni ife tonse.

33 Potero, popeza anakwezedwa ndi dzanja Lamanja la Mulungu, nalandira kwa Atate lonjezano la Mzimu Woyera, anatsanulira ici, cimene inu mupenya nimumva.

34 Pakuti Davine sanakwera Kumwamba ai; koma anena yekha, Ambuye anati kwa Mbuye wanga, Khalani ku dzanja lamanja langa,

35 Kufikira ndikaike adani ako copondapo mapazi ako.

36 Pamenepo lizindikiritse ndithu banja liri lonse la Israyeli, kuti Mulungu anamuyesa Ambuye ndi Kristu, Yesu amene inu munampacika.

37 Koma pamene anamva ici, analaswa mtima, natitu kwa Petro ndi atumwi enawo, Tidzacita ciani, amuna inu, abale?

38 Koma Petro anati kwa iwo, Lapani, batizidwani yense wa inu m'dzina la Yesu Kristu kuloza ku cikhululukiro ca macimo anu; ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.

39 Pakuti lonjezano 1 liri kwa inu, ndi kwa ana anu, 2 ndi kwa onse akutali, 3 onse amene Ambuye Mulungu wathu adzaitana.

40 Ndipo ndi mau ena ambiri anacita umboni, nawadandaulira iwo, nanena, Mudzipulumutse kwa mbadwo uno wokhotakhota.

41 Pamenepo iwo amene analandira mau ace anabatizidwa; ndipo anaonjezedwa tsiku lomwelo anthu ngati zikwi zitatu.

42 Ndipo 4 anali cikhalire m'ciphunzitso ca atumwi ndi m'ciyanjano, m'kunyema mkate ndi mapemphero.

43 Koma panadza mantha pa anthu onse; ndipo 5 zozizwa ndi zizindikilo zambiri zinacitika ndi atumwi.

44 Ndipo onse akukhulupira anali pamodzi, 6 nakhala nazo zonse zodyerana.

45 Ndipo zimene anali nazo, ndi cuma cao, anazigulitsa, nazigawira kwa onse, monga momwe yense anasowera.

46 Ndipo tsiku ndi tsiku 7 anali cikhalire ndi mtima umodzi m'Kacisi, ndipo ananyema mkate kunyumba kwao, nalandira cakudya ndi msangalalo, ndi mtima woona;

47 nalemekeza Mulungu, 8 ndi kukhala naco cisomo ndi anthu onse. Ndipo 9 Ambuye anawaonjezera tsiku ndi tsiku amene akuti apulumutsidwe.

3

1 Koma Petro ndi Yohane analikukwera kunka kuKacisi pa ora lakupembedza, ndilo lacisanu ndi cinai.

2 Ndipo munthu wina wopunduka miyendo cibadwire ananyamulidwa, amene akamuika masiku onse pa khomo la Kacisi lochedwa Lokongola, kuti apemphe zaulere kwa iwo akulowa m'Kacisi;

3 ameneyo, pakuona Petro ndi Yohane akuti alowe m'Kacisi, anapempha alandire caulere.

4 Ndipo Petro, pompenyetsetsa iye pamodzi ndi Yohane, anati, Tiyang'ane ife.

5 Ndipo iye anabvomereza iwo, nalingirira kuti adzalandira kanthu.

6 Koma Petro anati, Siliva ndi golidi ndiribe; koma cimene ndiri naco, ici ndikupatsa, M'dzina la Yesu Kristu Mnazarayo, yenda,

7 Ndipo anamgwira Iye ku dzanja lace lamanja, namnyamutsa; ndipo pomwepo mapazi ace ndi mfundo za kumapazi zinalimbikitsidwa.

8 Ndipo anazunzuka, naimirira, nayenda; ndipo analowa pamodzi nao m'Kacisi, nayenda, nalumpha, nayamika Mulungu.

9 Ndipo anthu onse anamuona iye, alikuyenda ndi kuyamika Mulungu;

10 namzindikira iye, kuti ndiye amene anakhala pa Khomo Lokongola la Kacisi: ndipo anadzazidwa ndi kudabwa ndi kuzizwa pa ici cidamgwera.

11 Koma m'mene anagwira Petro ndi Yohane, anawathamangira pamodzi anthu onse ku khumbi lochedwa la Solomo, alikudabwa ndithu.

12 Koma m'mene Petro anaciona, anayankha kwa anthu, Amuna inu a Israyeli, muzizwa naye bwanji ameneyo? kapena mutipenyetsetsa ife bwanji, monga ngati tamyendetsa iye ndi mphamvu ya ife eni, kapena ndi cipembedzo cathu?

13 Mulungu wa Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo, Mulungu wa makolo athu, analemekeza Mwana wace Yesu; amene, inu munampereka ndi kumkaniza pa Pilato, poweruza iyeyu kummasula.

14 Koma inu munakaniza Woyera ndi Wolungamayo, ndipo munapempha kuti munthu wambanda apatsidwe kwa inu,

15 ndipo munamupha Mkulu wa moyo; amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa; za ici ife tiri mboni.

16 Ndipo pa cikhulupiriro ca m'dzina lace dzina lacelo linalimbikitsa iye amene mumuona, nimumdziwa; ndipo cikhulupiriro ciri mwa iye cinampatsa kucira konse kumeneku pamaso pa inu nonse.

17 Ndipo tsopano, abale, ndidziwa kuti munacicita mosadziwa, monganso akulu anu.

18 Koma zimene Mulungu analalikiratu m'kamwa mwa aneneri onse, kuti adzamva kuwawa Kristu, iye anakwaniritsa cotero.

19 Cifukwa cace lapani, bwererani kuti afafanizidwe macimo anu, kotero kuti zidze nyengo zakutsitsimutsa zocokera ku nkhope ya Ambuye;

20 ndipo atume amene anaikidwa kwa inu, Kristu Yesu;

21 amene thambo la kumwamba liyenera kumlandira kufikira nthawi zakukonzanso zinthu zonse, zimene Mulunguanalankhula za izo m'kamwa mwa aneneri ace oyera ciyambire.

22 Mosetu anati, Mbuye Mulungu adzaukitsira inu mneneri mwa abale anu, ngati ine; mudzamvera iye m'zinthu ziri zonse akalankhule nanu.

23 Ndipo kudzali, kuti wamoyo ali yensesamvera mneneri ameneyu, adzasakazidwa konse mwa anthu.

24 Koma angakhale aneneri onse kuyambira Samuelindi akumtsatira, onse amene analankhula analalikira za masiku awa.

25 Inu ndinu ana a aneneri, ndi a panganolo Mulungu anapangana ndi makolo anu ndi kunena kwa Abrahamu, Ndipo mu mbeu yako mafuko onse a dziko adzadalitsidwa.

26 Kuyambira ndi inu, Mulungu, ataukitsa Mwana wace, anamtuma kukudalitsani inu, ndi kukubwezani yense ku zoipa zace.

4

1 Koma m'mene analikulankhula ndi anthu, ansembe ndi mdindo wa kuKacisi ndi Asaduki anadzako,

2 obvutika mtima cifukwa anaphunzitsa anthuwo, nalalikira mwa Yesu kuuka kwa akufa.

3 Ndipo anawathira manja, nawaika m'ndende kufikira m'mawa; pakuti mpa madzulo pamenepo.

4 Koma ambiri a iwo amene adamva mau anakhulupira; ndipo ciwerengero ca amuna cinali ngati zikwi zisanu.

5 Koma panali m'mawa mwace, anasonkhana pamodzi m'Yerusalemu oweruza, ndi akulu, ndi alembi;

6 ndi Anasi mkulu wa ansembe, ndi Kayafa, ndi Yohane, ndi Alesandro, ndi onse amene anali a pfuko la mkulu waansembe.

7 Ndipo m'mene anawaimika pakati, anafunsa kuti, Ndi mphamvu yanji, kapena m'dzina lanji, mwacita ici inu?

8 Pamenepo Petro, wodzala ndi Mzimu Woyera anati kwa iwo, Oweruza a anthu inu, ndi akulu,

9 ngati ife lero tiweruzidwa cifukwa ca nchito yabwino ya pa munthu wodwala, ndi maciritsidwe ace,

10 zindikirani inu nonse, ndi anthu onse a Israyeli, kuti m'dzina la Yesu Kristu Mnazarayo, amene inu munampacika pamtanda, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa, mwa Iyeyu munthuyu aimirirapo pamaso panu, wamoyo.

11 Iye ndiye mwalawo woyesedwa wopanda pace ndi inu omanga nyumba, umene unayesedwa mutu wa pangondya.

12 Ndipo palibe cipulumutso mwa wina yense, pakuti palibe dzina lina pansi pa thambo la kumwamba, lopatsidwa mwa anthu, limene tiyenera kupulumutsidwanalo.

13 Koma pakuona kulimbika mtima kwa Petro ndi Yohane, ndipo pozindikira kuti ndiwo anthu osaphunzira ndi opulukira, anazizwa ndipo anawazindikira, kuti adakhala pamodzi ndi Yesu.

14 Ndipotu pakuona munthu wociritsidwayoalikuimirira pamodzi nao, analibe kanthu kakunena kotsutsa.

15 Koma pamene anawalamulira iwo acoke m'bwalo la akulu, ananena wina ndi mnzace,

16 kuti, Tidzawacitira ciani anthu awa? pakutitu caoneka kwa onse akukhala m'Yerusalemu kuti cizindikilo cozindikirika cacitidwa ndi iwo, ndipo sitingathe kukana.

17 Komatu tiwaopse asalankhulenso m'dzina ili kwa munthu ali yense, kuti cisabukenso kwa anthu.

18 Ndipo anawaitana, nawalamulira kuti asanene konse kapena kuphunzitsa m'dzina la Yesu.

19 Koma Petro ndi Yohane anayankha nati kwa iwo, Weruzani, ngati nkwabwino pamaso pa Mulungu kumvera inu koposa Mulungu;

20 pakuti sitingatheife kuleka kulankhula zimene tinaziona ndi kuzimva.

21 Koma m'mene anawaopsanso anawamasula, osapeza kanthu kakuwalanga, cifukwa ca anthu; pakuti onse analemekeza Mulungu cifukwa ca comwe cidacitika.

22 Pakuti anali wa zaka zace zoposa makumi anai munthuyo, amene cizindikilo ici cakumciritsa cidacitidwa kwa iye.

23 Ndipo m'mene anamasulidwa, anadza kwa anzao a iwo okha, nawauza ziri zonse oweruza ndi akulu adanena nao.

24 Ndipo m'mene adamva, anakweza mau kwa Mulungu ndi mtima umodzi, nati, Mfumu, Inu ndinu wolenga thambo la kumwamba ndi dziko, ndi nyanja, ndi zonse ziri m'menemo;

25 amene mwa Mzimu Woyera, pakamwa pa kholo lathu Davine mtumiki wanu, mudati, Amitundu anasokosera cifukwaciani? Nalingirira zopanda pace anthu?

26 Anadzindandalitsa mafumu a dziko, Ndipo oweruza anasonkhanidwa pamodzi, Kutsutsana ndi Ambuye, ndi Kristu wace.

27 Pakuti zoonadi anasonkhanidwa m'mudzi muno Herode, ndi Pontiyo Pilato yemwe pamodzi ndi amitundu ndi anthu a Israyeli kumcitira coipa Mwana wanu wopatulika Yesu amene munamdzoza;

28 kuti acite ziri zonse dzanja lanu ndi uphungu wanu zidaweruziratu zicitike.

29 Ndipo tsopano Ambuye, penyani mau ao akuopsa, ndipo patsani kwa akapolo anu alankhule mau anu ndi kulimbika mtima konse,

30 m'mene mutambasula dzanja lanu kukaciritsa; ndi kuti zizindikilo ndi zozizwa zicitidwe mwa dzina la Mwana wanu wopatulika Yesu.

31 Ndipo m'mene adapemphera iwo, panagwedezeka pamalo pamene adasonkhanirapo; ndipo anadzazidwa onse ndi Mzimu Woyera, nalankhula mau a Mulungu molimbika mtima.

32 Ndipo unyinji wa iwo akukhulupira anali wa mtima umodzi ndi moyo umodzi; ndipo sananena mmodzi kuti kanthu ka cuma anali naco ndi kace ka iye yekha; koma anali nazo zonse zodyerana.

33 Ndipo atumwi anacita umboni ndi mphamvu yaikulu za kuuka kwa Ambuye Yesu; ndipo panali cisomo cacikuru pa iwo onse.

34 Pakuti mwa iwo munalibe wosowa; 1 pakuti onse amene anali nayo minda, kapena nyumba, anazigulitsa nabwera nao malonda ace a izo adazigulitsa,

35 2 nawaika pa mapazi a atumwi; ndipo anagawira yense monga kusowakwace.

36 Ndipo Yosefe, wochedwa ndi atumwi Bamaba (ndilo losandulika mwana wa cisangalalo), Mlevi, pfuko lace la ku Kupro,

37 pokhala nao munda, anaugulitsa, nabwera nazo ndalama zace, 3 naziika pa mapazi a atumwi.

5

1 Koma munthu wina dzina lace Hananiya pamodzi ndi Safira mkazi wace,

2 anagulitsa cao, napatula pa mtengo wace, mkazi yemwe anadziwa, natenga cotsala, naciika pa mapazi a atumwi.

3 Koma Petro anati, Hananiya, Satana anadzaza mtima wako cifukwa ninji kudzanyenga Mzimu Woyera, ndi kupatula pa mtengo wace wa mundawo?

4 Pamene unali nao, sunali wako kodi? ndipo pamene unaugulitsa sunali m'manja mwako kodi? bwanji cinalowa ici mumtima mwako? sunanyenga anthu, komatu Mulungu.

5 Koma Hananiya pakumva mau awa anagwa pansi namwalira: ndipo mantha akuru anagwera onse akumvawo.

6 Ndipo ananyamuka anyamata, namkulunga, namnyamula, naturuka naye, namuika.

7 Koma atapita monga maora atatu, ndipo mkazi wace, wosadziwa cidacitikaco, analowa.

8 Ndipo Petro ananena naye, Undiuze, ngati munagulitsa mundawo pa mtengo wakuti. Ndipo ananena, Inde, wakuti.

9 Koma Petro anati kwa iye, Munapangana pamodzi bwanji kuyesa Mzimu wa Ambuye? Taona, mapazi ao a iwo amene anaika mwamuna wako ali pakhomo, ndipo adzakunyamula kuturuka nawe.

10 Ndipo anagwa pansi pomwepo pa mapazi ace, namwalira; ndipo analowa anyamatawo, nampeza iye wafa, ndipo anamnyamula kuturuka naye, namuika kwa mwamuna wace.

11 Ndipo anadza mantha akuru pa Mpingo wonse, ndi pa onse akumvaizi.

12 Ndipo mwa manja aatumwi zizindikilo ndi zozizwa zambiri zinacitidwa pa anthu; ndipo anali onse ndi mtima umodzi m'khumbi la Solomo.

13 Koma palibe mmodzi wa otsalawo analimba mtima kuphatikana nao; komatu anthu anawakuzitsa;

14 ndipo makamaka anaonjezedwa kwa Ambuye okhulupirira ambiri, ndiwo amuna ndi akazi;

15 kotero kuti ananyamulanso naturuka nao odwala Ifumakwalala, nawaika pamakama ndi pamphasa, kuti, popita Petro, ngakhale cithunzi cace cigwere wina wa iwo.

16 Komanso unasonkhana pamodzi unyinji wa anthu ocokera ku midzi yozungulira Yerusalemu, alikutenga odwala, ndi obvutika ndi mizimu yonyansa; ndipo anaciritsidwa onsewa.

17 Koma anauka mkulu wa ansembe ndi onse amene anali naye, ndiwo a cipatuko ca Asaduki, nadukidwa,

18 nathira manja atumwi, nawaika m'ndende ya anthu wamba.

19 Koma mngelo wa Ambuye anatsegula pakhomo pa ndende usiku, nawaturutsa, nati,

20 Pitani, ndipo imirirani, nimulankhule m'Kacisi kwa anthu onse mau a Moyo umene.

21 Ndipo atamva ici, analowa m'Kacisi mbanda kuca, naphunzitsa. Koma anadza mkulu wa ansembe ndi iwo amene analinaye, nasonkhanitsa a bwalo la akuru, ndi akulu onse a ana a Israyeli, natuma kundende atengedwe ajawo.

22 Koma anyamata amene adafikako sanawapeza m'ndende, ndipo pobwera anafotokoza,

23 nanena, Nyumba yandende tinapeza citsekere, ndi alonda alikuimirira pamakomo; koma pamene tinatsegula sitinapezamo mmodzi yense.

24 Koma m'mene anamva mau awa mdindo wa Kacisi ndi ansembe akulu anathedwa nzeru ndi iwo aja, kuti ici cidzatani.

25 Ndipo anadza wina nawafotokozera, kuti, Taonani, amuna aja mudawaika m'ndende ali m'Kacisi, alikuimirira ndi kuphunzitsa anthu.

26 Pamenepo anacoka mdindo pamodzi ndi anyamata; nadza nao, koma osawagwiritsa, pakuti anaopa anthu, angaponyedwe miyala.

27 Ndipo m'mene adadza nao, anawaika pa bwalo la akuru. Ndipo anawafunsa mkuru wa ansembe,

28 nanena, Tidakulamulirani cilamulire, musaphunzitsa kuchula dzina ili; ndipo taonani, mwadzaza Yerusalemu ndi ciphunzitso canu, ndipo mufuna kutidzetsera ife mwazi wa munthu uja.

29 Ndipo anayankha Petro ndi atumwi, nati, Tiyenera kumvera Mulungu koposa anthu.

30 Mulungu wa makolo athu anaukitsa Yesu, amene munamupha inu, ndi kumpacika pamtengo.

31 Ameneyo Mulungu anamkweza ndi dzanja lace lamanja, akhale Mtsogoleri ndi Mpulumutsi, kuti apatse kwa Israyeli kulapa, ndi cikhululukiro ca macimo.

32 Ndipo ife ndife mboni za zinthu izi; Mzimu Woyeranso, amene Mulungu anapatsa kwa iwo akumvera iye.

33 Koma m'mene anamva iwo analaswa mtima, nafuna kuwapha.

34 Koma ananyamukapo wina pa bwalo la akuru, ndiye Mfarisi, dzina lace Gamaliyeli, mphunzitsi wa cilamulo, wocitidwa ulemu ndi anthu onse, nalamula kuti atumwiwo akhale kunja pang'ono.

35 Ndipo anati kwa iwo, Amuna inu a Israyeli, kadzicenjerani nokha za anthu awa, cimene muti muwacitire.

36 Pakuti asanafike masiku ana anauka Teuda, nanena kuti ali kanthu iye mwini; amene anthu anaphatikana naye, ciwerengero cao ngati mazana anai; ndiye anaphedwa; ndi onse amene anamvera iye anamwazika, napita pacabe.

37 Atapita ameneyo, anauka Yuda wa ku Galileya, masiku a kulembedwa, nakopa anthu amtsate. Iyeyunso anaonongeka, ndi onse amene anamvera iye anabalalitsidwa.

38 Ndipo tsopano ndinena ndi inu, Lekani anthu amenewa, nimuwalole akhale; pakuti ngati uphungu umene kapena nchito iyi icokera kwa anthu, idzapasuka;

39 koma ngati icokera kwa Mulungu simungathe kuwapasula; kuti kapena mungapezeke otsutsana ndi Mulungu.

40 Ndipo anabvomerezana ndi iye; ndipo m'meheadaitana atumwi, anawakwapula nawalamulira asalankhule kuchula dzina la Yesu, ndipo anawamasula.

41 Pamenepo ndipo anapita kucokera ku bwalo la akuru, 1 nakondwera kuti anayesedwa oyenera kunyozedwa cifukwa ca dzinalo.

42 Ndipo masiku onse, m'Kacisi ndi m'nyumba, 2 sanaleka kuphunzitsa ndi kulalikira Kristu Yesu.

6

1 Koma masiku awo, pakucurukitsa ophunzira, kunauka cidandaulo, Aheleniste kudandaula pa Ahebri, popeza amasiye ao anaiwalika pa citumikiro ca tsiku ndi tsiku.

2 Ndipo khumi ndi awiriwo anaitana unyinji wa ophunzira, nati, Sikuyenera kuti ife tisiye mau a Mulungu ndi kutumikira podyerapo.

3 Cifukwa cace, abale, yang'anani mwa inu amuna asanu ndi awiri a mbiri yahwino, odzala ndi Mzimu ndi nzeru, amene tikawaike asunge nchito iyi.

4 Koma ife tidzalimbika m'kupemphera, ndi kutumikira mau.

5 Ndipo mau amene anakonda unyinji wonse; ndipo anasankha Stefano, ndiye munthu wodzala ndi cikhulupiriro ndi Mzimu Woyera, ndi Filipo, ndi Prokoro, ndi Nikanora ndi Timo, ndi Parmena, ndi Nikolao, ndiye wopinduka wa ku Antiokeya:

6 amenewo anawaika pamasopa atumwi; ndipo m'mene adapemphera, anaika manja pa iwo.

7 Ndipo mau a Mulungu anakula; ndipo ciwerengero ca akuphunzira cidacurukatu ku Yerusalemu; ndipo khamu lalikuru la ansembe linamvera cikhulupiriroco.

8 Ndipo Stefano, wodzala ndi cisomo ndi mphamvu, anacita zozizwa ndi zizindikilo zazikuru mwa anthu.

9 Koma anauka ena a iwo ocokera m'sunagoge wa Alibertino, ndi Akurenayo, ndi Aalesandreyo, ndi mwa iwo a ku Kilikiya ndi ku Asiya, natsutsana ndi Stefano.

10 Ndipo sanathe kuilaka nzeru ndi Mzimu amene analankhula naye.

11 Pamenepo anafuna anthu akumpitira pansi, ndi kuti, Tidamumva iye alikunenera Mose ndi Mulungu mau amwano.

12 Ndipo anautsa anthu, ndi akuru, ndi alembi, namfikira, namgwira iye, nadza naye ku bwalo la akulu,

13 naimika mboni zonama, zakunena, Munthu ameneyo saleka kunenera malo oyera amene, ndi cilamulo;

14 pakuu tinamumva iye alikunena, kuti, Yesu Mnazarayo amene adzaononga malo ano, nadzasanduliza miyambo imene Mose anatipatsa.

15 Ndipo anampenyetsetsa onse akukhala m'bwalo la akulu, naona nkhope yace ngati nkhope ya mnaelo.

7

1 Ndipo mkulu wa ansembe anati, Zitero izi kodi?

2 Ndipo Stefano anati, Amuna inu, abale, ndi atate, tamverani. Mulungu wa ulemerero anaonekera kwa kholo lathu Abrahamu, pokhala iye m'Mesopotamiya, asanayambe kukhala m'Harana;

3 nati kwa iye, Turuka ku dziko lako ndi kwa abale ako, ndipo tiye ku dziko limene ndidzakusonyeza iwe.

4 Pamenepo anaturuka m'dziko la Akaldayo namanga m'Harana: ndipo, kucokera kumeneko, atamwalira atate wace, Mulungu anamsuntha alowe m'dziko lino, m'mene mukhalamo tsopano;

5 ndipo sanampatsa colowa cace m'menemo, ngakhale popondapo phazi lace iai; ndipo anamlonjezera iye kuti adzampatsa ili, likhale lace, ndi la mbeu yace yomtsatira, angakhale analibe mwana pamenepo.

6 Koma Mulungu analankhula cotero, kuti mbeu yace idzakhala alendo m'dziko la eni, ndipo adzawacititsa ukapolo, nadzawacitira coipa, zaka mazana anai.

7 Ndipo mtundu amene udzawayesa akapolo, ndidzauweruza Ine, anatero Mulungu; ndipo zitapita izi adzaturuka, nadzanditumikira Ine m'malo muno.

8 Ndipo anaiupatsa iye cipangano ca mdulidwe; ndipo kotero Abrahamu anabala Isake, namdula tsiku lacisanu ndi citatu; ndi Isake anabala Yakobo, ndi Yakobo anabala makolo akulu aja khumi ndi awiri.

9 Ndipo makolo akuluwa podukidwa naye Yosefe, anamgulitsa amuke naye ku Aigupto; ndipo Mulungu anali naye,

10 namlanditsa iye m'zisautso zace zonse, nampatsa cisomo ndi nzeru pamaso pa Farao mfumu ya ku Aigupto; ndipo anamuika iye kazembe wa pa Aigupto ndi pa nyumba yace yonse.

11 Koma inadza njala pa Aigupto ndi Kanani lonse, ndi cisautso cacikuru; ndipo sanapeza cakudya makolo athu.

12 Koma pakumva Yakobo kuti muli tirigu m'Aigupto, anatuma makolo athu ulendo woyamba,

13 Ndipo pa ulendo waciwiri Y osefe anazindikirika ndi abale ace; ndipo pfuko la Yosefe linaonekera kwa Farao.

14 Ndipo Yosefe anatumiza, naitana Yakobo atate wace, ndi a banja lace lonse, ndiwo anthu makumi asanu ndi awiri mphambu asanu.

15 Ndipo Yakobo anatsikira ku Aigupto; ndipo anamwalira, iye ndi makolo athu;

16 ndipo anawanyamula kupita nao ku Sukemu, nawaika m'manda amene Abrahamu adagula ndi mtengo wace wa ndalama kwa ana a Emori m'Sukemu.

17 Koma m'mene inayandikira nthawi ya lonjezo limene Mulungu adalonjezana ndi Abrahamu, anthuwo anakula nacuruka m'Aigupto,

18 kufikira inauka mfumu yina pa Aigupto, imene siinamdziwa Yosefe.

19 Imeneyo inacenjerera pfuko lathu, niwacitira coipa makolo athu, niwatayitsa tiana tao, kuti tingakhale ndi moyo.

20 Nyengo yomweyo anabadwa Mose, ndiye wokoma ndithu; ndipo anamlera miyezi itatu m'nyumba ya atate wace:

21 ndipo pakutayika iye, anamtola mwana wamkazi wa Farao, namlera akhale mwana wace.

22 Ndipo Moseanaphunzira nzeru zonse za Aaigupto; nali wamphamvu m'mau ace ndi m'nchito zace.

23 Koma pamene zaka zace zinafikira ngati makumi anai, kunalowa mumtima mwace kuzonda abale ace ana a Israyeli,

24 Ndipo pakuona wina woti alikumcitira cotpa, iye anamcinjiriza, nambwezera cilango wozunzayo, nakantha M-aigupto.

25 Ndipo anayesa kuti abale ace akazindikira kuti Mulungu alikuwapatsa cipulumutso mwa dzanja lace; koma sanazindikira.

26 Ndipo m'mawa mwace anawaonekera alikulimbana ndeu, ndipo anati awateteze, ayanjanenso, nati, Amuna inu, muli abale; mucitirana coipa bwanji?

27 koma iye wakumcitira mnzace coipa anamkankha, nati, Wakuika iwe ndani mkulu ndi wotiweruzira?

28 1 Kodi ufuna kundipha ine, monga muja unapha M-aigupto dzulo?

29 2 Ndipo Mose anathawa pa mau awa, nakhala mlendo m'dziko la Midyani; kumeneko anabala ana amuna awiri.

30 Ndipo 3 zitapita zaka makumi anai, anamuonekera mngelo m'cipululu ca Sina, m'lawi la mota wa m'citsamba.

31 4 Koma Mose pakuona, anazizwa pa coonekaco; ndipo pakuyandikira iye kukaona, kunadza mau a Ambuye,

32 5 akuti, Ine ndine Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, ndi wa Isake, ndi wa Yakobo. Ndipo Mose ananthunthumira, osalimbika mtima kupenyetsako.

33 6 Ndipo Ambuye anati kwa iye, Masula nsapato ku mapazi ako; pakuti pa malo amene upondapo mpopatulika.

34 7 Kuona ndaona coipidwa naco anthu anga ali m'Aigupto, ndipo a amva kubuula kwao; ndipo ndatsika kuwalanditsa; ndipo tsopano tiye kuno, ndikutume ku Aigupto

35 Mose uyu amene anamkana, ndi kuti, Wakuika iwe ndani mkuru ndi woweruza? ameneyo Mulungu anamtuma akhale mkuru, ndi mombolo, ndi dzanja la mngelo womuonekera pacitsamba.

36 Ameneyo anawatsogolera, naturuka nao 8 atacita zozizwa ndi zizindikilo m'Aigupto, ndi m'Nyanja Yofiira, ndi m'cipululu zaka makumi anai.

37 Uyu ndi Mose uja adati kwa ana a Israyeli, 9 Mulungu adzakuutsirani Mneneri wa mwa abale anu, monga ine.

38 10 Uyu ndiye amene anali mu Mpingo m'cipululu pamodzi ndi mngelo wakulankhula naye m'phiri la Sina, ndi makolo athu: amene analandira maneno amoyo akutipatsa ife;

39 amene makolo athu sanafuna kumvera iye, koma anamkankha acoke, nabwerera m'mbuyo mumtima mwao ku Aigupto,

40 11 nati ndi Aroni, Tipangireni milungu yotitsogoleraife; pakuti Mose uja, amene anatiturutsa m'Aigupto, sitidziwa comwe camgwera.

41 Ndipo 12 anapanga mwana wa ng'ombe masiku omwewo, nabwera nayo nsembe kwa fanolo, nasekerera ndi nchito za manja ao.

42 Koma 13 Mulungu anatembenuka, nawapereka iwo atumikire gulu la kumwamba; monga kwalembedwa m'buku laaneneri, 14 Kodi mwapereka kwa Ine nyama zophedwa ndi nsembe Zaka makumi anai m'cipululu, nyumba ya Israyeli inu?

43 15 Ndipo munatenga cihema ca Moloki, Ndi nyenyezi ya mulungu Refani, Zithunzizo mudazipanga kuzilambira; Ndipo ndidzakutengani kunka nanu m'tsogolo mwace mwa Babulo.

44 Cihema ca umboni cinali ndi makolo athu m'cipululu, monga adalamula iye wakulankhula ndi Mose, 16 acipange ici monga mwa cithunzico adaciona.

45 17 Cimenenso makolo athu akudza m'mbuyo, analowa naco ndi Y oswa polandira iwo zao za amitundu, 18 amene Mulungu anawaingitsa pamaso pa makolo athu, kufikira masiku a Davine;

46 amene anapeza cisomo pamaso pa Mulungu, napempha kuti apeze mokhalama Mulungu wa Yakobo.

47 Kama 19 Solomo anammangira nyumba.

48 Komatu 20 Wamwambamwambayo sakhala m'nyumba zomangidwa ndi manja; monga mneneri anena,

49 21 Thambo la kumwamba ndilo mpando wacifumu wanga, Ndi dziko lapansi copondapo mapazi anga: Mudzandimangira nyumba yotani? ati Ambuye; Kapena malo a mpumulo wanga ndi otani?

50 Silinapanga dzanja langa zinthu izi zonse kodi?

51 22 Ouma khosi ndi osadulidwa mtima ndi makutu inu, mukaniza Mzimu Woyera nthawi zonse; monga anacita makolo anu, momwemo inu.

52 23 ndiye yani wa aneneri makolo anu sanamzunza? ndipo anawapha iwo amene anaonetseratu za kudzakwace kwa Wolungamayo; wa iye amene mwakhala tsopano akumpereka ndi akumupha;

53 inu amene munalandira cilamulo 24 monga cidaikidwa ndi angelo, ndipo simunacisunga.

54 Koma pakumva izi analaswa mtima, namkukutira mano.

55 Koma iye, 25 pokhala wodzala ndi Mzimu Woyera, anapenyetsetsa Kumwamba, naona ulemerero wa Mulungu, ndi Yesu alikuimirira pa dzanja lamanja la Mulungu,

56 nati, Taonani, 26 ndipenya m'Mwamba motseguka, ndi Mwana wa munthu alikuimirira pa dzanja lamanja la Mulungu.

57 Koma anapfuula ndi mau akuru, natseka m'makutu mwao, namgumukira iye ndi mtima umodzi;

58 ndipo 27 anamtaya kunja kwa mudzi, namponya miyala; ndipo 28 mbonizo zinaika zobvala zao pa mapazi a mnyamata dzina lace Saulo.

59 Ndipo anamponya miyala Stefano, alikuitana Ambuye, ndi kunena, 29 Ambuye Yesu, landirani mzimu wanga.

60 Ndipo m'mene anagwada pansi, anapfuula ndi mau akuru, 30 Ambuye, musawaikire iwo cimo ili. Ndipo m'mene adanena ici, anagona tulo.

8

1 Ndipo Saulo analikubvomerezana nao pa imfa yace. Ndipo tsikulo kunayamba kuzunza kwakukuru pa Mpingo unali m'Yerusalemu; ndipo anabalalitsidwa onse m'maiko a Yudeya ndi samariya, koma osati atumwi ai.

2 Ndipo anamuika Stefano anthu opembedza, namlira maliro akuru.

3 Ndipo Saulo anapasula Mpingo, nalowa m'nyumba m'nyumba, nakokamo amuna ndi akazi, nawaika m'ndende.

4 Pamenepo ndipo iwo akubalalitsidwa anapitapita nalalikira mauwo.

5 Ndipo Filipo anatsikira ku mudzi wa ku Samarlya, nawalalikira iwo Kristu.

6 Ndipo makamuwo ndi mtima umodzi anasamalira zonenedwa ndi Filipo, pamene anamva, napenya zizindikilo zimene anazicita.

7 Pakuti ambiri a iwo akukhala nayo mizimu yonyansa inawaturukira, yopfuula ndi mau akuru; ndipo ambiri amanjenje, ndi opunduka, anaciritsidwa.

8 Ndipo panakhala cimwemwe cacikuru m'mudzimo.

9 Koma panali munthu dzina lace Simoni amene adacita matsenga m'mudzimo kale, nadabwitsa anthu a Samariya, ndi kunena kuti iye yekha ndiye munthu wamkuru;

10 ameneyo anamsamalira onsewo, kuyambira wamng'ono kufikira wamkuru, ndi kunena, Uyu ndiye mphamvu ya Mulungu, yonenedwa Yaikuru.

11 Ndipo anamsamalira iye, popeza nthawi yaikuru adawadabwitsa iwo ndi matsenga ace.

12 Koma pamene anakhulupirira Filipo wakulalikira Uthenga Wabwinowa Ufumu wa Mulungu ndi dzina la Yesu Kristu, anabatizidwa, amuna ndi akazi.

13 Ndipo Simoni mwini wace anakhulupiranso: ndipo m'mene anabatizidwa, anakhalira ndi Filipo; ndipo pakuona zizindikilo ndi mphamvu zazikuru zirikucitika, anadabwa.

14 Koma pamene atumwi a ku Yerusalemu anamva kuti Samariya adalandira mau a Mulungu, anawatumizira Petro ndi Yohane;

15 amenewo, m'mene adatsikirako, anawapempherera, kuti alandire Mzimu Woyera:

16 pakuti kufikira pamenepo nkuti asanagwe pa wina mmodzi wa iwo; koma anangobatizidwam'dzina la Ambuye Yesu.

17 Pamenepo anaika manja pa iwo, ndipo analandira Mzimu Woyera.

18 Koma pakuona Simoni kuti mwa kuika manja a atumwi anapatsidwa Mzimu Woyera, anawatengera ndalama,

19 nanena, Ndipatseni inenso ulamuliro umene, kuti amene ali yense ndikaika manja pa iye, alandire Mzimu Woyera.

20 Koma Petro anati kwa iye, Ndalama yako itayike nawe, cifukwa unalingirira kulandira mphatso ya Mulungu ndi ndalama.

21 Ulibe gawo kapena colandira ndi mau awa; pakuti mtima wako suli wolunjika pamaso pa Mulungu.

22 Cifukwa: cace lapa coipa calm ici, pemphera Ambuye, kuti kapena akukhululukire iwe colingiriraca mtima wako.

23 Pakuti ndiona kuti wagwidwa ndi ndulu yowawa ndi nsinga ya cosalungama.

24 Ndipo Simoni anayankha nati, Mundipempherere ine kwa Ambuye kuti zisandigwere izi mwanenazi.

25 Pamenepo iwo, atatha kucita umboni ndi kulankhula mau a Ambuye, anabwerakunkaku Yerusalemu, nalalikira Uthenga Wabwi no ku midzi yambirl ya Asamariya.

26 Koma mngelo wa Ambuye analankhula ndi Filipo, nanena, Nyamuka, nupite mbali ya kumwela, kutsata njira yotsika kucokera ku Yerusalemu kunka ku Gaza; ndiyo ya cipululu.

27 Ndipo ananyamuka napita; ndipo taona munthu wa ku Aitiopiya, mdindo wamphamvu wa Kandake, mfumu yaikazi ya Aaitiopiya, ndiye wakusunga cuma cace conse, amene anadza ku Yerusalemu kudzapemphera;

28 ndipo analinkubwerera, nalikukhala pa gareta wace, nawerenga mneneri Yesaya.

29 Ndipo Mzimu anati kwa Filipo, Yandikira, nudziphatike ku gareta uyu.

30 Ndipo Filipo anamthamangira, namva iye alikuwerenga Yesaya mneneri, ndipo anati, Kodi muzindikira cimene muwerenga?

31 Koma anati, Ndingathe bwanji, popanda munthu wonditsogolera ine? ndipo anapempha Filipo akwere nakhale naye.

32 Koma palembo pamene analikuwerengapo ndipo. Ngati nkhosa anatengedwa kukaphedwa, Ndi monga mwana wa nkhosa ali du pamaso pa womsenga, Kotero sanatsegula pakamwa pace:

33 M'kucepetsedwa kwace ciweruzo cace cinacotsedwa; Mbadwo wace adzaubukitsa ndani? Cifukwa wacotsedwa kudziko moyo wace.

34 Ndipo mdindoyo anayankha Filipo, nati, Ndikupempha, mneneri anena ici za yani? za yekha, kapena za wina?

35 Ndipo Filipo anatsegula pakamwa pace, nayamba pa lembo ili, nalalikira kwa iye Yesu.

36 Ndipo monga anapita paniire pao, anadza ku madzi akuti; ndipo mdindoyo anati, Taonapo madzi; cindiletsa ine ciani ndisabatizidwe? [

37 ]

38 Ndipo anamuuza kuti aimitse gareta; ndipo anatsikira onse awiri kumadzi, Filipo ndi mdindoyo; ndipoanambatiza iye.

39 Ndipo pamene anakwera kururuka m'madzi, Mzimu wa Ambuye anakwatula Filipo; ndipo mdindo sanamuonanso, pakuti anapita njira yace wokondwera.

40 Koma Filipo anapezedwa ku Azotu; ndipo popitapitaanalalikira Uthenga Wabwino m'midzi yonse, kufikira anadza iye ku Kaisareya.

9

1 Koma Saulo, wosaleka kupumira pa akuphunzira a Ambuye kuopsya ndi kupha, ananka kwa mkulu wa ansembe,

2 napempha kwa iye akalata akunka nao ku Damasiko kumasunagoge, kuti akapeza ena otsata Njirayo, amuna ndi akazi, akawatenge kudza nao omangidwa ku Yerusalemu.

3 Ndipo poyenda ulendo wace, kunali kuti iye anayandikira Damasiko: ndipo mwadzidzidzi kudawala momzingira kuunika kocokera kumwamba;

4 ndipo anagwa pansi, namva mau akunena naye, Saulo, Saulo, Undilondalonderanji?

5 Koma anati, Ndiouyani Mbuye? Ndipo anati, Ndine Yesu amene umlondalonda;

6 komatu, uka, nulowe m'mudzi, ndipo kudzanenedwa kwa iwe cimene uyenera kucita.

7 Ndipo amunawo akumperekeza iye anaima du, atamvadi mau, koma osaona munthu.

8 Ndipo Saulo anauka; koma potseguka maso ace, sanapenya kanthu; ndipo anamgwira dzanja, namtenga nalowa naye ni'Damasiko.

9 Ndipo anakhala masiku atatu wosaona, ndipo sanadya kapena kumwa.

10 Koma ku Damasiko kunali wophunzira wina dzina lace Hananiya; ndipo Ambuye anati kwa iye m'masomphenya, Hananiya. Ndipo anati, Ndiri pano, Ambuye,

11 Ndipo Ambuye anati kwa iye, Tauka, pita ku khwalala lochedwa Lolunjika, ndipo m'nyumba ya Yuda ufunse za munthu dzina lace Saulo, wa ku Tariso: pakuti taona, alikupemphera

12 ndipo anaona mwamuna dzina, lace Hananiya, alikulowa, namuika manja, kuti apenyenso.

13 Ndipo Hananiya anayankha nati, Ambuye ndamva ndi ambiri za munthu uyu kuti anacitiradi coipa oyera mtima anu m'Yerusalemu;

14 ndi kuti pane ali nao ulamuliro wa kwa ansembe akulu wakumanga onse akuitana pa dzina lanu.

15 Koma Ambuye anat kwa iye, Pita; pakuti iye ndiye cotengera canga cosankhika, cakunyamula dzina langa pamaso pa amitundu ndi mafumu ndi ana a Israyeli;

16 pakuti Ine ndidzamuonetsa iye zinthu zambirl ayenera iye kuzimva kuwawa cifukwaca dzina langa.

17 Ndipo anacoka Hananiya, nalowa m'nyumbayo; ndipo anaika manja ace pa iye, nati, Saulo, mbale, Ambuye wandituma ine, ndiye Yesu amene anakuonekerani pa njira wadzerayo, kuti upenyenso, ndi kudzazidwa ndi Mzimu Woyera.

18 Ndipo pomwepo padagwa kucoka m'maso mwace ngati mamba, ndipo anapenyanso;

19 ndipo ananyamuka nabatizidwa; ndipo analandira cakudya, naona naco mphamvu. Ndipo anakhala pamodzi ndi akuphunzira a ku Damasiko masiku ena.

20 Ndipo pomwepo m'masunagoge analalikira Yesu, kuti iye ndiye Mwana wa Mulungu.

21 Ndipo onse amene anamva anadabwa, nanena, Suyu iye amene anaononga m'Yerusalemu onse akuitana pa dzina ili? Ndipo wadza kuno kudzatero, kuti amuke nao omangidwa kwa ansembe akuru.

22 Koma Saulo anakula makamaka mumphamvu, nadodometsa Ayuda akukhala m'Damasiko, nawatsimikizira kuti ameneyo ndi Kristu.

23 Ndipo atapita masiku ambiri, Ayuda anapangana kuti amuphe iye;

24 koma ciwembu cao cinadziwika ndi Saulo. Ndipo anadikiranso pazipata usana ndi usiku kuti amuphe;

25 koma ophunzira ace anamtenga usiku, nampyoletsa palinga, namtsitsa ndi mtanga,

26 Koma m'mene anafika ku Yerusalemu, anayesa kudziphatika kwa ophunzira; ndipo anamuopa iye onse, osakhulupirira kuti ali wophunzira.

27 Koma Bamaba anamtenga, napita naye kwa atumwi, nawafotokozera umo adaonera Ambuye m'njira, ndi kuti analankhula naye, ndi kuti m'Damasiko adanena molimbika mtima m'dzina la Yesu.

28 Ndipo anali pamodzi nao, nalowa naturuka ku Yerusalemu,

29 nanena molimbika mtima m'dzina la Ambuye; ndipotu analankhula natsutsana ndi Aheleniste; koma anayesayesa kumupha iye.

30 Koma m'mene abale anacidziwa, anapita naye ku Kaisareya, namtumiza acokeko kunka ku Tariso.

31 Pamenepo ndipo Mpingo wa m'Yudeya Ionse ndi Galileya ndi Samariya unali nao mtendere, nukhazikika; ndipo unayenda m'kuopa kwa Ambuye ndi m'citonthozo ca Mzimu Woyera, nucuruka.

32 Koma kunali, pakupita Petro ponse ponse, anatsikiranso kwa oyera mtima akukhalaku Luda.

33 Ndipo anapeza kumeneko munthu dzina lace Eneya, amene anagonera pamphasa zaka zisanu ndi zitatu; amene anagwidwa manjenje.

34 Ndipo Petro anati kwa iye, Eneya, Yesu Kristu akuciritsa iwe; uka, yalula mphasa yako. Ndipo anauka pomwepo.

35 Ndipo anamuona iye onse akukhala ku Luda ndi ku Sarona, natembenukira kwa Ambuye amenewa.

36 Koma m'Yopa munali wophunzira dzina lace Tabita, ndilo kunena Dorika; mkazi ameneyo anadzala ndi nchito zabwino ndi zacifundo zimene anazicita.

37 Ndipo kunali m'masiku awa, kuti anadwala iye, namwalira; ndipo atamsambitsa iye anamgoneka m'cipinda ca pamwamba.

38 Ndipo popeza Luda ndi pafupi pa Yopa, m'mene anamva ophunzirawo kuti Petro anali pomwepo, anamtumizira anthu awiri, namdandaulira, Musacedwa mudze kwa ife.

39 Ndipo Petro anayamuka, napita nao. M'mene anafikako, anapita naye ku cipinda ca pamwamba; ndipo amasiye onse anaimirirapo pali iye, nalira, namuonetsa maraya ndizobvala zimene Dorika adasoka, pamene anali nao pamodzi.

40 Koma Petro anawaturutsa onse, nagwada pansi, napemphera; ndipo potembenukira kumtembo anati, Tabita, uka. Ndipo anatsegula maso ace; ndipo pakuona Petro, anakhala tsonga.

41 Ndipo Petro anamgwiradzanja, namnyamutsa; ndipo m'mene adaitana oyera mtima ndi amasiye, anampereka iye wamoyo.

42 Ndipo kudadziwika ku Yopa konse: ndipo ambiri anakhulupirira Ambuye.

43 Ndipo kunali, kuti anakhala iye m'Yopa masiku ambiri ndi munthu Simoni wofufuta zikopa.

10

1 Ndipo kunali munthu ku Kaisareya, dzina lace Komeliyo, kenturiyo wa gulu lochedwa la Italiya,

2 ndiye munthu wopembedza, ndi wakuopa Mulungu ndi banja lace lonse, amene anapatsa anthu zacifundo zambiri, napemphera Mulungu kosaleka.

3 Iye anapenya m'masomphenya poyera, mngelo wa Mulungu alinkudza kwa iye, ngati ora lacisanu ndi cinai la usana, nanena naye, Komeliyo.

4 Ndipo pompenyetsetsa iye ndi kuopa, anati, Nciani, Mbuye? Ndipo anati kwa iye, Mapemphero ako ndi zacifundo zako zinakwera zikhala cikumbutso pamaso pa Mulungu.

5 Ndipo tsopano tumiza amuna ku Y opa, aitane munthu Simoni, wochedwanso Petro;

6 acerezedwa iye ndi wina Simoni wofufuta zikopa, nyumba yace iri m'mbali mwa nyanja.

7 Ndipo m'mene atacoka mngelo amene adalankhula naye, anaitana anyamata ace awiri, ndi msilikari wopembedza, wa iwo amene amtumikira kosaleka;

8 ndipo m'mene adawafotokozerazonse, anawatuma ku Yopa.

9 Koma m'mawa mwace, pokhala paulendo pao iwowa, m'mene anayandikira mudzi, Petro anakwera pachindwi kukapemphera, ngati pa ora lacisanu ndi cimodzi; ndipo anagwidwa njala, nafuna kudya;

10 koma m'mene analikumkonzera cakudya kudamgwera ngati kukomoka;

11 ndipo anaona pathambo padatseguka, ndi cotengera cirinkutsika, conga ngati cinsaru cacikuru, cogwiridwa pa ngondya zace zinai, ndi kutsikira padziko pansi;

12 m'menemo munali nyama za miyendo inai za mitundu yonse, ndi zokwawa za padziko ndi mbalame za m'mlengalenga.

13 Ndipo anamdzera mau, Tauka, Petro; ipha, nudye.

14 Koma Petro anati, Iaitu, Mbuye; pakuti sindinadya ine ndi kale lonse kanthu wamba ndi konyansa.

15 Ndipo mau anamdzeranso nthawi yaciwiri, Cimene Mulungu anayeretsa, usaciyesa cinthu wamba.

16 Ndipo cinacitika katatu ici; ndipo pomwepo cotengeraco cinatengedwa kunka kumwamba.

17 Ndipo pokayika-kayika Petro mwa yekha ndi kuti masomphenya adawaona akuti ciani, taonani, amuna aja otumidwa ndi Komeliyo, atafunsira nyumba ya Simoni, anaima pa cipata,

18 ndipo anaitana nafunsa ngati Simoni, wochedwanso Petro, acerezedwako.

19 Ndipo m'mene Petro analingirira za masomphenya, Mzimu ananena naye, Taona, amuna atatu akufuna iwe.

20 Komatu tauka, nutsike, ndipo upite nao, wosakayika-kayika; pakuti ndawatuma ndine.

21 Ndipo Petro anatsikira kwa anthuwo, nati, Taonani, ine ndine amene mumfuna; cifukwa cace mwadzera nciani?

22 Ndipo anati, Komeliyo kenturiyoyo, munthu wolungama ndi wakuopa Mulungu, amene mtundu wonse wa Ayuda umcitira umboni, anacenjezedwa ndi mngelo woyera kuti atumize nakuitaneni mumuke ku nyumba yace, ndi kummvetsa mau anu.

23 Pamenepo anawalowetsa nawacereza. Ndipo m'mawa mwace ananyamuka naturuka nao, ndi ena a abale a ku Yopaanamperekezaiye.

24 Ndipo m'mawa mwace analowa m'Kaisareya, Koma Komeliyo analikudikira iwo, atasonkhanitsa abale ace ndi mabwenzi ace eni eni.

25 Ndipo panali pakulowa Petro, Komeliyo anakomana naye, nagwa pa mapazi ace, namlambira.

26 Koma Petro anamuutsa iye, nanena, Nyamuka; inenso ndine munthu.

27 Ndipo pakukamba naye, analowa, napeza ambiri atasonkhana;

28 ndipo anati kwa iwo, Mudziwa inu nokha kuti sikuloledwa kwa munthu Myuda adziphatike kapena kudza kwa munthu wa mtundu wina; koma Mulungu anandionetsera ine ndisanenere ali yense ali munthu wamba kapena wonyansa;

29 cifukwa cacenso ndinadza wosakana, m'mene munatuma kundiitana. Pamenepo ndifunsa, mwandiitaniranji?

30 Ndipo Komeliyo anati, Atapita masiku anai, kufikira monga ora ili, ndinalikupemphera m'nyumba yanga pa ora lacisanu ndi cinai; ndipo taonani, padaimirira pamaso panga munthu wobvala cobvala conyezimira,

31 nati Komeliyo, lamveka pemphero lako, ndi zopereka zacifundo zako zakumbukika pamaso pa Mulungu.

32 Cifukwa cace tumiza anthu ku Yopa, akaitane Simoni amene anenedwanso Petro; amene acerezedwa m'nyumba ya Simoni wofufuta zikopa, m'mbali mwa nyanja.

33 Pamenepo ndinatumiza kwa inu osacedwa; ndipo mwacita bwino mwadza kuno, Cifukwa cace taonani tiri tonse pano pamaso pa Mulungu, kumva zonse Ambuye anakulamulirani.

34 Ndipo Petro anatsegula pakamwa pace, nati: Zoona ndizinkidira kuti Mulungu alibe tsankhu;

35 koma m'mitundu yonse, wakumuopa iye ndi wakucita cilungamo alandiridwa naye.

36 Mau amene anatumiza kwa ana a Israyeli, akulalikira Uthenga Wabwino wa mtendere mwa Yesu Kristu (ndiye Ambuye wa onse)

37 mauwo muwadziwa inu, adadzawo ku Yudeya lonse, akuyamba ku Galileya, ndi ubatizo umene Yohane anaulalikira;

38 za Yesu wa ku Nazarete, kuti Mulungu anamdzoza iye ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu; amene anapitapita nacita zabwino, naciritsa onse osautsidwa ndi mdierekezi, pakuti Mulungu anali pamodzi ndi iye.

39 Ndipo ife ndife mboni zazonse adazicita m'dzikola Ayuda ndim'Yerusalemu; amenenso anamupha, nampacika pamtengo,

40 Ameneyo, Mulungu anamuukitsa tsiku lacitatu, nalola kuti aonetsedwe,

41 si kwa anthu onse ai, koma kwa mboni zosankhidwiratu ndi Mulungu, 1 ndiwo ife amene tinadya ndi kumwa naye pamodzi, atauka iye kwa akufa.

42 Ndipo 2 anatilamulira ife tilalikire kwa anthu, ndipo ticite umboni kuti 3 Uyu ndiye amene aikidwa ndi Mulungu akhale woweruza amoyo ndi akufa.

43 4 Ameneyu aneneri onse amcitira umboni, kuti onse akumkhulupirira iye adzalandira cikhululukiro ca macimo ao, mwa dzina lace.

44 Petro ali cilankhulire, 5 Mzimu Woyera anagwa pa onse akumva mauwo.

45 Ndipo 6 anadabwa okhulupirirawo akumdulidwe onse amene anadza ndi Petro, cifukwa pa 7 amitundunso panathiridwa mphatso ya Mzimu Woyera.

46 Pakuti anawamva iwo alikulankhula ndi malilime, ndi kumkuza Mulungu. Pamenepo Petro anayankha,

47 Kodi pali munthu akhoza kuletsa madzi, kuti asabatizidwe awa, amene alandira Mzimu Woyera 8 ngatinso ife?

48 Ndipo analamulira iwo 9 abatizidwe m'dzina la Yesu Kristu, Pamenepo anampempha iye atsotse masiku.

11

1 Koma atumwi ndi abale akukhala m'Yudeya anamva kuti amitundunso adalandira mau a Mulungu.

2 Ndipo pamene Petro adakwera kudza ku Yerusalemu, iwo a kumdulidwe anatsutsana naye,

3 nanena kuti, Munalowa kwa anthu osadulidwa, ndi kudya nao.

4 Koma Petro anayamba kuwafotokozera cilongosolere, nanena,

5 Ndinali ine m'mudzi wa Yopa ndi kupemphera; ndipo m'kukomoka ndinaona masomphenya, cotengera cirikutsika, ngati cinsaru cacikuru cogwiridwa pa ngondya zace zinai; ndi kutsika kumwamba, ndipo cinadza pali ine;

6 cimeneco ndidacipenyetsetsa ndinacilingirira, ndipo ndinaona nyama za miyendo inai za padziko ndi zirombo, ndi zokwawa, ndi mbalame za m'mlengalenga.

7 Ndipo ndinamvanso mau akunena ndi ine, Tauka Petro; ipha, nudye.

8 Koma ndinati, Iaitu, Ambuye; pakuti kanthu wamba, kapena konyansa sikanalowe m'kamwa mwanga ndi kale lonse.

9 Koma mau anayankha nthawi yaciwiri oturuka m'mwamba, Cimene Mulungu anaciyeretsa, usaciyesera cinthu wamba.

10 Ndipo ici cinacitika katatu; ndipo zinakwezekanso zonse kumwamba.

11 Ndipo taonani, pomwepo amuna atatu anaima pa khomo la nyumba m'mene munali ife, anatumidwa kwa ine ocokera ku Kaisareya.

12 Ndipo Mzimu anandiuza ndinke nao, wosasiyanitsa konse. Ndipo abale awa asanu ndi mmodzi anandiperekezanso anamuka nane; ndipo tinalowa m'nyumba ya munthuyo;

13 ndipo anatiuza ife kuti adaona mngelo wakuimirira m'nyumba yace, ndi kuti, Tumiza anthu ku Yopa, akaitane Simoni, wonenedwanso Petro;

14 amene adzalankhula nawe mau, amene udzapulumutsidwa nao iwe ndi apabanja ako onse.

15 Ndipo m'mene ndinayamba kulankhula, Mzimu Woyera anawagwera, monga anatero ndi ife poyamba paja.

16 Ndipo ndinakumbuka mau a Ambuye, kuti ananena, Yohanetu anabatiza ndi madzi; koma inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.

17 Ngati tsono Mulungu anawapatsa iwo mphatso yomweyi yonga ya kwa ife, pamene tinakhulupirira Ambuye Yesu Kristu, ndine yani kuti ndingathe kuletsa Mulungu?

18 Ndipo pamene anamva izi, anakhala du, nalemekeza Mulungu, ndi kunena, a Potero Mulungu anapatsa kwa amitundunso kutembenukira mtima kumoyo.

19 Pamenepo iwotu, akubalalika cifukwa ca cisautsoco cidadza pa Stefano, anafikira ku Foinike, ndi Kupro, ndi Antiokeya, osalankhula mau kwa wina yense koma kwa Ayuda okha.

20 Koma panali ena mwa iwo, amuna a ku Kupro, ndi Kurene, amenewo, m'mene adafika ku Antiokeya, analankhula ndi Ahelene, ndi kulalikira Uthenga Wabwino wa Ambuye Yesu.

21 Ndipo dzanja la Ambuye linali nao; ndi unyinji wakukhulupira unatembenukira kwa Ambuye.

22 Ndipo mbiri yao inamveka m'makutu a Mpingo wakukhala m'Yerusalemu; ndipo anatuma Bamaba apite kufikira ku Antiokeya;

23 ameneyo, m'mene anafika, naona cisomo ca Mulungu, anakondwa; ndipo anawandandaulira onse, kuti atsimikize mtima kukhalabe ndi Ambuye;

24 cifukwa anali munthu wabwino, ndi wodzala ndi Mzimu Woyera ndi cikhulupiriro: ndipo khamu lalikuru lidaonjezeka kwa Ambuye.

25 Ndipo anaturuka kunka ku Tariso kufunafuna Saulo;

26 ndipo m'mene anampeza, anadza naye ku Antiokeya. Ndipo kunali, kuti caka conse anasonkhana pamodzi mu Mpingo, naphunzitsa anthu aunyinji; ndipo ophunzira anayamba kuchedwa Akristu ku Antiokeya.

27 Koma masiku awa aneneri anatsika ku Yerusalemu kudza ku Antiokeya.

28 Ndipo anyanamuka mmodzi wa iwo, dzina lace Agabo, nalosa mwa Mzimu, kuti padzakhala njala yaikulu pa dziko lonse lokhalamo anthu; ndiyo idadza masiku a Klaudiyo.

29 Ndipo akuphunzira, yense monga anakhoza, anatsimikiza mtima kutumiza zothandiza abale akukhala m'Yudeya;

30 iconso anacita, natumiza kwa akulu mwa dzanja la Bamaba ndi Saulo.

12

1 Koma nyengo imeneyo Herode mfumu anathira manja ena a m'Eklesia kuwacitira zoipa.

2 Ndipo adapha ndi lupanga Yakobo a mbale wa Yohane.

3 Ndipo pakuona kuti kudakondweretsa Ayuda, anaonjezapo nagwiranso Petro. Ndipo awo ndi masiku a mkate wopanda cotupitsa.

4 Ndipo m'mene adamgwira, anamuika m'ndende, nampereka kwa magulu anai a alonda, lonse anai anai, amdikire iye; ndipo anafuna kumturutsa kudza naye kwa anthu atapita Paskha.

5 Pamenepo ndipo Petro anasungika m'ndende; koma Eklesia anampempherera iye kwa Mulungu kosalekeza.

6 Ndipo pamene Herode anati amturutse, usiku womwewo Petro analikugona pakati pa asilikari awiri, womangidwa ndi maunyolo awiri; ndipo alonda akukhalapakhomoanadikira ndende.

7 Ndipo taonani, mngelo wa Ambuye anaimirirapo, ndipo kuunika kunawala mokhalamo iye; ndipo anakhoma Petro m'nthiti, namuutsa iye, nanena, Tauka msanga, Ndipo maunyolo anagwa kucoka m'manja mwace.

8 Ndipo mngelo anati kwa iye, Dzimangire m'cuuno, numange nsapato zako. Nacita cotero. Ndipo ananena naye, Pfunda cobvala cako, nunelitsate ine.

9 Ndipo anaturuka, namtsata; ndipo sanadziwa kuti ncoona cocitidwa ndi mngelo, koma anayesa kuti alikuona masomphenya.

10 Ndipo m'mene adapitirira podikira poyamba ndi paciwiri, anadza ku citseko cacitsulo cakuyang'ana kumudzi; cimene cidawatsegukira cokha; ndipo anaturuka, napitirira khwalala limodzi; ndipo pomwepo mngelo anamcokera.

11 Ndipo Petro atatsitsimuka, anati, Tsopano ndidziwa zoona, kuti Ambuye anatuma mngelo wace nandilanditsa ine m'dzanja la Herode, ndi ku cilingiriro conse ca anthu a Israyeli.

12 Ndipo m'mene adalingirirapo, anadza ku nyumba ya Marlys amace wa Yohane wonenedwanso Marko; pamenepo ambiri adasonkhana pamodzi, ndipo analikupemphera,

13 Ndipo m'mene anagogoda pa citseko ca pakhomo, linadza kudzabvomera buthu, dzina lace Roda.

14 Ndipo pozindikira mau ace a Petro, cifukwa ca kukondwera sanatsegula pakhomo, koma anathamanga nalowanso, nawauza kuti Petro alikuima pakhomo.

15 Koma anati kwa iye, Wamisala iwe. Ndipo analimbika ndi kunena kuti nkutero. Ndipo ananena, Ndiye mngelo wace.

16 Koma Petro anakhala cigogodere; ndipo m'mene adamtsegulira, anamuona iye, nadabwa.

17 Koma m'mene adawatambasulira dzanja akhale cete, anawafotokozera umo, adamturutsira Ambuye m'ndende. Ndipo anati, Muwauze Yakobo ndi abale izi, Ndipo anaturuka napita kwina.

18 Koma kutaca, panali phokoso lalikuru mwa asilikari, Petro wamuka kuti.

19 Ndipo pamene Herode adamfunafuna, wosampeza, anafunsitsa odikira nalamulira aphedwe. Ndipo anatsika ku Yudeya kunka ku Kaisareya, nakhalabe kumeneko.

20 Koma Herode anaipidwa nao a ku Turo ndi Sidoni; ndipo anamdzera iye ndi mtima umodzi, ndipo m'mene adakopa Blasto mdindo wa mfumu, anapempha mtendere, popeza dziko lao linapeza zakudya zocokera ku dziko la mfumu.

21 Ndipo tsiku lopangira Herode anabvala zobvala zacifumu, nakhala pa mpando wacifumu, nawafotokozera iwo mau a pabwalo.

22 Ndipo anthu osonkhanidwawo anapfuula, Ndiwo mau a Mulungu, si a munthu ai.

23 Ndipo pomwepo mngelo wa Ambuye anamkantha, cifukwa sanampatsa Mulungu ulemerero; ndipo anadyedwa ndi mphutsi, natsirizika.

24 Koma mau a Mulungu anakula, nacurukitsa.

25 Ndipo Bamaba ndi Saulo anabwera kucokera ku Yerusalemu m'mene adatsiriza utumiki wao, natenga Yohane wonenedwanso Marko amuke nao.

13

1 Ndipo kunali aneneri ndi aphunzioo ku Antiokeya mu Mpingo wa komweko, ndiwo Barnaba, ndi Sumeoni, wonenedwa Nigeri, ndi Lukiya wa ku Kurene, Manayeni woleredwa pamodzi ndi Herode ciwangaco, ndi Saulo.

2 Ndipo pa kutumikira Ambuye iwowa, ndi kusala cakudya, Mzimu Woyera anati, Mundipatulire Ine Bamaba ndi Saulo ku nchito imene odinawaitanirako.

3 Pamenepo, m'mene adasala cakudya ndi kupemphera ndi kuika manja pa iwo, anawatumiza amuke.

4 Pamenepo iwo, otumidwa ndi Mzimu Woyera, anatsikira ku Selukeya; ndipo pocokerapo anapita m'ngalawa ku Kupro.

5 Ndipo pokhala ku Salami, analalikira mau a Mulungu m'masunagoge a Ayuda; ndipo anali nayenso Yohane mnyamata wao.

6 Ndipo m'mene anapitirira cisumbu conse kufikira Pafo, anapezapo munthu watsenga, mneneri wonyenga, ndiye Myuda, dzina lace Baryesu;

7 ameneyo anali ndi kazembe Sergio Paulo, ndiye munthu wanzeru. Yemweyo anaitana Barnaba ndi Saulo, nafunitsa kumva mau a Mulungu.

8 Koma Elima watsengayo (pakuti dzina lace litera posandulika) anawakaniza, nayesa kupatutsa kazembe asakhulupire.

9 Koma Saulo, ndiye Paulo, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anampenyetsetsa iye,

10 nati, Wodzala ndi cinyengo conse ndi cenjerero lonse, iwe, mwana wa mdierekezi, mdani wa cilungamo conse, kodi sudzaleka kuipsa njira zolunjika za Ambuye?

11 Ndipo tsopano, taona, dzanja la Ambuye liri pa iwe, ndipo udzakhala wakhungu wosapeoya dzuwa nthawi, Ndipo pomwepo lidamgwera khungu ndi mdima; ndipo anamukamoka oaf una wina womgwira dzanja.

12 Pamenepo kazembe, pakuona cocitikacoanakhulupira, nadabwa naco ciphunzitso ca Ambuye.

13 Ndipo atamasula kucokera ku Pafo a ulendo wace wa Paulo anadza ku Perge wa ku Pamfuliya; koma Yohane anapatukana nao nabwerera kunka ku Yerusalemu.

14 Koma iwowa, atapita pocokera ku Perge anafika ku Antiokeya wa m'Pisidiya; ndipo analowa m'sunagoge tsiku la Sabata, nakhala pansi.

15 Ndipo m'mene adatha kuwerenga cilamulo ndi aneneri akulu a sunagoge anatuma wina kwa iwo, ndi kunena, Amuna inu, abale, ngati muli nao mau akudandaulira anthu, nenani.

16 Ndipo Paulo ananyamuka, nakodola ndi dzanja, nati, Amuna a Israyeli, ndi inu akuopa Mulungu, mverani.

17 Mulungu wa anthu awa Israyeli anasankha makolo athu, nakweza anthuwo pakugonerera iwo m'dziko la Aigupto, ndipo ndi dzanja lokwezeka anawaturutsa iwo m'menemo.

18 Ndipo monga nthawi ya zaka makumi anai anawalekerera m'cipululu.

19 Ndipo m'mene adaononga mitundu ya anthu isanu ndi iwiri m'Kanani, anawapatsa colowa dziko lao, monga zaka mazana anai kudza makumi asanu;

20 ndipo zitatha izi anawapatsa oweruza kufikira Samueli mneneriyo.

21 Ndipo kuyambira pamenepo anapempha mfumu; ndipo Mulungu anawapatsa Sauli mwana wa Kisi, munthu wa pfuko la Benjamini, zaka makumi anai.

22 Ndipo m'mene atamcotsa iye, anawautsira Davine akhale mfumu yao; amenenso anamcitira umboni, nati, Ndapeza Davine, mwana wa Jese, munthu wa pamtima panga, amene adzacita cifuniro canga conse.

23 Wocokera mu mbeu yace Mulungu, monga mwa lonjezano, anautsira Israyeli Mpulumutsi, Yesu;

24 Yohane atalalikiratu, asanafike iye, ubatizo wa kulapa kwa anthu onse a Israyeli.

25 Ndipo pakukwaniritsa njira yace Yohane, ananena, Muyesa kuti ine ndine yani? Ine sindine iye. Koma taonani, akudza wina wonditsata ine, amene sindiyenera kummasulira nsapato za pa mapazi ace.

26 Amuna, abale, ana a mbadwa ya Abrahamu, ndi iwo mwa inu akuopa Mulungu, kwa ife atumidwa mau a cipulumutso ici.

27 Pakuti iwo akukhala m'Yerusalemu, ndi akulu ao, popeza sanamzindikira iye, ngakhale mau a aneneri owerengedwa masabata onse, anawakwaniritsa pakumtsutsa.

28 Ndipo ngakhale sanapeza cifukwa ca kumphera, anapempha Pilato kuti aphedwe.

29 Ndipo atatsiriza zonse zolembedwa za iye, anamtsitsa kumtengo, namuika m'manda.

30 Koma Mulungu anamuukitsa iye kwa akufa;

31 ndipo 1 anaonekera masiku ambiri ndi iwo amene anamperekeza iye pokwera ku Yerusalemu kucokera ku Galileya, amenewo ndiwo akumcitira umboni tsopano kwa anthu.

32 Ndipo ife tikulalikirani inu Uthenga Wabwino wa 2 lonjezano locitidwa kwa makolo;

33 kuti Mulungu analikwaniritsa ili kwa ana athu pakuukitsa Yesu; monganso mulembedwa m'Salmo laciwiri, Iwe ndiwe Mwana wanga, lero ndakubala.

34 Ndipo kuti anamuukitsa iye kwa akufa, wosabweranso kueibvundi, anateropo, 3 Ndidzakupatsani inu madalitso oyera ndi okhulupirika a Davine.

35 Cifukwa anenanso m'Salmo lina, 4 Simudzapereka Woyera wanu aone cibvundi.

36 Pakutitu, Davine, m'mene adautumikira uphungu wa Mulungu m'mbadwo mwace mwa iye yekha, anagona tulo, naikidwa kwa makolo ace, naona cibvundi;

37 koma iye amene Mulungu anamuukitsa sanaona cibvundi.

38 Potero padziwike ndi inu amuna abale, 5 kuti mwa iye cilalikidwa kwa inu cikhululukiro ca macimo;

39 ndipo 6 mwa iye yense wokhulupira ayesedwa wolungama kumcotsera zonse zimene simunangathe kudzicotsera poyesedwa wolungama ndi cilamulo ca Mose.

40 Cifukwa cace penyerani, kuti cingadzere inu conenedwa ndi anenenwo:

41 7 Taona ni, opeputsa inu, zizwani, kanganukani; Kuti ndigwiritsa nchito Ine masikuanu, Nchito imene simudzaikhulupira wina akakuuzani.

42 Ndipo pakuturuka iwo anapempha kuti alankhule naonso mau awa Sabata likudzalo.

43 Ndipo m'mene anthu a m'sunagoge anabalalika, Ayuda ambiri ndi akupinduka opembedza anatsata. Paulo ndi Bamaba; amene, polankhula nao, 8 anawaumiriza akhale m'cisomo ca Ambuye.

44 Ndipo Sabata linalo udasonkhana pamodzi ngati mudzi wonse kumva mau a Mulungu.

45 Koma Ayuda, pakuona makamu a anthu, anadukidwa, natsutsana nazo zolankhulidwa ndi Paulo, nacita mwano.

46 Ndipo Paulo ndi Bamaba analimbika mtima ponena, nati, 9 Kunafunika kuti mau a Mulungu ayambe alankhulidwe kwa inu. 10 Popeza muwakankha, nimudziyesera nokha osayenera moyo wosatha, taonani, titembenukira kwa amitundu.

47 Pakuti kotero anatilamulira Ambuye ndi kuti, 11 Ndakuika iwe kuunika kwa amitundu, Kuti udzakhala iwe cipulumutso kufikira malekezero a dziko.

48 Ndipo pakumva ici amitundu anakondwera, nalemekeza mau a Mulungu; ndipo anakhulupira onse amene anaikidwiratu ku moyo wosatha.

49 Ndipo mau a Ambuye anabukitsidwa m'dziko lonse.

50 Koma Ayuda anakakamiza akazi opembedza ndi omveka, ndi akulu a mudziwo, 12 nawautsira cizunzo Paulo ndi Bamaba, ndipo ana wapitikitsaiwom'malire ao.

51 Koma iwo, 13 m'mene adawasansirapfumbi la ku mapazi ao anadza ku Ikoniyo,

52 Ndipo 14 akuphunzira anadzazidwa ndi cimwemwe ndi Mzimu Woyera.

14

1 Ndipo kunali pa Ikoniyo kuti analowa pamodzi m'sunagoge wa Ayuda, nalankhula kotero, kuti khamu lalikuru la Ayuda ndi Ahelene anakhulupira.

2 Koma Ayuda osamvefa anautsa mitima ya Ahelene kuti aipse abale athu.

3 Cifukwa cace anakhala nthawi yaikuru nanenetsa zolimba mtima mwa Ambuye, amene anacitira umboni mau a cisomo cace, napatsa zizindikiro ndi zozizwa kuti zicitidwe ndi manja ao.

4 Ndipo khamu la mudziwo linagawikana; ena analindi Ayuda, komaena anali ndi atumwi.

5 Ndipo pamene panakhala cigumukiro ca Ahelene ndi ca Ayuda ndi akuru ao, ca kuwacitira cipongwe ndi kuwaponya miyala,

6 iwo anamva, nathawira ku midzi ya Lukaoniya, Lustra ndi Derbe, ndi dziko lozungulirapo:

7 kumeneko ndiko Uthenga Wabwino.

8 Ndipo pa Lustra panakhala munthu wina wopanda mphamvu ya m'mapazi mwace, wopunduka cibadwire, amene sanayenda nthawi zonse.

9 Ameneyo anamva Paulo alinkulankhula; ndipo Paulo pomyang'anitsa, ndi kuona kuti anali ndi cikhulupiriro colandira naco moyo,

10 anati ndi mau akuru, Taimirira. Ndipo iyeyu anazunzuka, nayenda.

11 Pamene makamu anaona cimene anacita Paulo, anakweza mau ao, nati m'cinenero ca Lukaoniya, Milungu yatsikira kwa ife monga anthu.

12 Ndipo anamucha Bamaba, Zeu; ndi Paulo, Herme, cifukwa anali wotsogola kunena.

13 Koma wansembe wa Zeu wa kumaso kwa mudzi, anadza nazo ng'ombe ndi maluwa kuzipata, nafuna kupereka nsembe pamodzi ndi makamu.

14 Pamene anamva atumwi Paulo ndi Bamaba, anang'amba zopfunda zao, natumphira m'khamu,

15 napfuula Dati, Anthuni, bwanji mucita zimenezi? ifenso tiri anthu a mkhalidwe wathu umodzimodzi ndi wanu, akulalikira kwa inu Uthenga Wabwino, wakuti musiye zinthu zacabe izi, nimutembenukire kwa Mulungu wamoyo, amene analenga zakumwamba ndi zapansi, ndi nyanja, ndi zonse ziri momwemo:

16 m'mibadwo, yakale iye adaleka mitundu yonse iyende m'njira mwao.

17 Koma sanadzisiyira iye mwini wopanda umboni, popeza anacita zabwino, nakupatsani inu zocokera kumwamba mvulaodi nyengoza zipatso, ndi kudzaza mitima yanu ndi cakudya ndicikondwero.

18 Pakunena izo, anabvutika pakuletsa makamu kuti asapereke nsembe kwa iwo.

19 Ndipo anafika kumeneko Ayuda kucokera ku Antiokeya ndi Ikoniyo; nakopa makamu, ndipo anamponya Paulomiyala, namguzira kunja kwa mudzi; namuyesa kuti wafa.

20 Koma pamene, anamzinga akuphunzirawo, anauka iye, nalowa m'mudzi; m'mawa mwace anaturuka ndi Bamaba kunka, ku Derbe.

21 Pamene analalikira Uthenga Wabwino pamudzipo, nayesa ambiri akuphunzira, anabwera ku Lustra ndi Ikoniyo ndi Antiokeya,

22 nalimbikitsa mitima ya akuphunzira, nadandauliraiwo kuti akhalebe m'cikhulupiriro, ndi kuti tiyenera kulowa m'ufumu wa Mulungu ndi zisautso zambiri.

23 Ndipo pamene anawaikira akuru mosankha mu Mpingo Mpingo, ndi kupemphera pamodzi ndi kusala kudya, anaikiza iwo kwa Ambuye amene anamkhulupirirayo.

24 Ndipo anapitirira pa Pisidiya, nafika ku Pamfuliya.

25 Ndipo atalankhula mau m'Perge, anatsikira ku Ataliya;

26 komweko anacoka m'ngalawa kunka ku Antiokeya, kumene anaikizidwa ku cisomo ca Mulungu ku Ilchito imene adaimarizayo,

27 Pamene anafika nasonkhanitsa Mpingo anabwerezanso zomwe Mulungu anacita nao, kuti anatsegulira amitundu pa khomo la cikhulupiriro.

28 Ndipo anakhala pamenepo ndi akuphunzira nthawi yaikuru.

15

1 Ndipo anadza ena akutsika ku Yudeya, nawaphunzitsa abale, nati, Mukapandakudulidwa monga mwambo wa Mose, simungathe kupulumuka.

2 Ndipo pamene Paulo ndi Bamaba anacitana nao makani ndi mafunsano, abale anapatula Paulo ndi Bamaba, ndi ena a iwo, kuti akwere kunka ku Yerusalemu kwa atumwi ndi akuru kukanena za funsolo.

3 Ndipo iwo anaperekezedwa ndi Mpingo, napita pa Foinike ndi Samariya, nafotokozera cisanduliko ca amitundu; nakondweretsa kwambiri abale onse.

4 Pamene anafika ku Yerusalemu, analandiridwa ndi Mpingo, ndi atumwi ndi akuru, ndipo anabwerezanso zonse zimene Mulungu anacita nao.

5 Koma anauka ena a mpatuko wa Afarisi okhulupira, nati, Kuyenera kuwadula iwo, ndi kuwauza kuti asunge cilamulo ca Mose.

6 Ndipo anasonkhana atumwi ndi akuru kuti anene za mlanduwo.

7 Ndipo pamene panali mafunsano ambiri, Petro anaimirira, nati kwa iwo, Abale, mudziwa kuti poyamba Mulungu anasankha mwa inu, kuti m'kamwa mwanga amitundu amve mau a Uthenga Wabwino, nakhulupire.

8 Ndipo Mulungu, amene adziwa mtima, anawacitira umboni; nawapatsa Mzimu Woyera, monga anatipatsa ife;

9 ndipo sanalekanitsa ife ndi iwo, nayeretsa mitima yao m'cikhulupiriro.

10 Nanga bwanji tsopano mulikumuyesa Mulungu, kuti muike pa khosi la akuphunzira gori, limene sanatha kunyamula kapena makolo athu kapena ife?

11 Koma tikhulupira tidzapulumuka mwa cisomo ca Ambuye Yesu Kristu, monga iwo omwe.

12 Ndipo khamu lonse linatonthola; ndipo anamvera Bamaba ndi Paulo alikubwerezanso zizindikiro ndi zozizwitsa zimene Mulungu anacita nao pa amitundu.

13 Pamene iwo anatonthola Yakobo anayankha, nati, Abale, mverani ine:

14 Sumeoni wabwereza kuti poyamba Mulungu anayang'anira amitundu, kuti atenge mwa iwo anthu a dzina lace.

15 Ndipo mau a aneneri abvomereza pamenepo; monga kunalembedwa,

16 Zikatha izo ndidzabwera, Ndidzamanganso cihema ca Davine, cimene cinagwa; Ndidzamanganso zopasuka zace, Ndipo ndidzaciimikanso:

17 Kuti anthu otsalira afunefune Ambuye, Ndi amitundu onse amene dzina langa linachulidwa pa iwo,

18 Ati Ambuye, amene azidziwitsa zinthu zonsezo ciyambire dzikolapansi.

19 Cifukwa cace ine ndiweruza, kuti tisabvute a mwa amitundu amene anatembenukira kwa Mulungu,

20 koma kuti tilembere kwa iwo, kuti asale zonyansa za mafano, ndi dama, ndi zopotola, ndi mwazi.

21 Pakuti Mose, kuyambira pa mibadwo yakale ali nao m'midzi yonse amene amlalikira, akuwerenga mau ace m'masunagoge masabata onse.

22 Pamenepo cinakomera atumwi ndi akuru ndi Eklesia yensekusankha anthu a m'gulu lao, ndi kuwatumiza ku Antiokeya ndi Paulo ndi Bamaba; ndiwo Yuda wochedwa Barsaba, ndi Sila, akuru a mwa abale; ndipo analembera mau natumiza ndi iwo:

23 Atumwi ndi abale akuru kwa abale a mwa amitundu a m'Antiokeya, ndi Suriya, ndi Kilikiya, tikulankhulani:

24 Popeza tamva kuti ena amene anaturuka mwa ife anakubvutani ndi mau, nasoceretsa mitima yanu; amenewo sitinawalamulira;

25 cinatikomera ndi mtima umodzi, tisankhe anthu, ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi okondedwa anthu Bamaba ndi Paulo,

26 anthu amene anapereka moyo wao cifukwa ca dzina la Yesu Kristu Ambuye wathu.

27 Tatumiza tsono Yuda ndi Sila, omwenso adzakuuzani ndi mau zinthu zomwezo.

28 Pakuti cinakomer a Mzimu Woyera ndi ife, kuti tisasenzetse inu cothodwetsa cacikuru cina coposa izi zoyenerazi;

29 kuti musale nsembe za mafano, ndi mwazi, ndi zopotola, ndi dama; ngati mudzisungitsa pa zimenezi, kudzakhala bwino kwa inu. Tsalani bwino.

30 Tsono pamene iwo anamuka anatsikira ku Antiokeya; ndipo anasonkhanitsa khamu, napereka kalatayo.

31 Pamene anawerenga, anakondwera cifukwa ca cisangalatso cace.

32 Ndipo Yuda ndi Sila, okhala eni okha aneneri, anasangalatsa abale ndi mau ambiri, nawalimbikitsa.

33 Pamene anakhala nthawi, abale analawirana nao ndi mtendere amuke kwa iwo amene anawatumiza. [

34 ]

35 Koma Paulo ndi Bamaba anakhalabe m'Antiokeya, nalinkuphunzitsa, ndi kulalikira mau a Ambuye pamodzi ndi ena ambiri.

36 Patapita masiku, Paulo anati kwa Bamaba, Tibwerenso, tizonde abale m'midzi yonse m'mene tinalalikiramo mau a Ambuye, tione mkhalidwe wao.

37 Ndipo Bamaba anafuna kumtenga Yohane uja, wochedwa Marko.

38 Koma sikunamkomera Paulo kumtenga iye amene anawasiya nabwerera pa Pamfuliya paja osamuka nao kunchito.

39 Ndipo panali kupsetsana mtima, kotero kuti analekana wina ndi mnzace; ndipo Bamaba anatenga Marko, nalowa n'ngalawa, nanka ku Kupro.

40 Koma Paulo anasankha Sila, namuka, woikizidwa ndi abale ku cisomo ca Ambuye.

41 Ndipo iye anapita kupyola pa Suriya ndi Kilikiya, nakhazikitsa Mipingo.

16

1 Ndipo anafikanso ku Derbe ndi Lustra; ndipo taonani, panali wophunzira wina pamenepo, dzina lace Timoteo, amace ndiye Myuda wokhulupira; koma atate wace ndiye Mhelene.

2 Ameneyo anamcitira umboni wabwino abale a ku Lustra ndi Ikoniyo.

3 Iyeyo Paulo anafuna kuti amuke naye, ndipo anamtenga, namdula, cifukwa ca Ayuda amene anakhala m'maikomo; pakuti onse anadziwa kuti atate wace anali Mhelene.

4 Pamene anapita kupyola pamidzi, anapereka kwa iwo malamulo awasunge, amene analamulira atumwi ndi akuru a pa Yerusalemu.

5 Kotero Mipingoyo inalimbikitsidwa m'cikhulupiriro, nacuruka m'ciwerengo cao tsiku ndi tsiku.

6 Ndipo anapita pa dziko la Frugiya ndi Galatiya, atawaletsa Mzimu Woyera kuti asalalikire mau m'Asiya; pamene anafika kundunji kwa Musiya,

7 anayesa kunka ku Bituniya; ndipo Mzimu wa Yesu sanawaloleza;

8 ndipo pamene anapita pambali pa Musiya, anatsikira ku Trowa.

9 Ndipo masomphenya anaonekera kwa Paulo usiku: Panali munthu wa ku Makedoniya alinkuimirira, namdandaulira kuti, Muolokere ku Makedoniya kuno, mudzatithangate ife.

10 Pamene anaona masomphenyawo, pomwepo tinayesa kuturukirakunka ku Makedoniya, poganizira kuti Mulungu anaitanira ife kulalikira Uthenga Wabwino kwa iwo.

11 Cotero tinacokera ku Trowa m'ngalawa, m'mene tinalunjikitsa ku Samotrake, ndipo m'mawa mwace ku Neapoli;

12 pocokera kumeneko tinafika ku Filipi, mudzi wa ku Makedoniya, waukuru wa m'dzikomo, wa miraga ya Roma; ndipojidagona momwemo masiku ena.

13 Tsiku la Sabata tinaturuka kumudzi kunka ku mbali ya mtsinje, kumene tinaganizira kuti amapempherako; ndipo tinakhala pansi ndi kulankhula ndi akazi amene adasonkhana,

14 Ndipo anatimva mkazi wina dzina lace Lidiya, wakugulitsa cibakuwa, wa ku mudzi wa Tiyatira, amene anapembedza Mulungu; mtima wace Ambuye anatsegula, kuti amvere zimene anazinena Paulo.

15 Pamene anabatizidwa iye ndi a pabanja pace anatidandaulira ife, kuti, Ngati mwandiyesera ine wokhulupirika kwa Ambuye, mulowe m'nyumba yanga, mugone m'menemo. Ndipo anatiumiriza ife.

16 Ndipo panali, pamene tinalinkunka kukapemphera, anakomana ndi ife namwali wina amene anali ndi mzimu wambwebwe, amene anapindulira ambuye ace zambiri pakubwebweta pace.

17 Ameneyo anatsata Paulo ndi ite, napfuula, kuti, Anthu awa ndi akapolo a Mulungu wa Kumwambamwamba amene akulalikirani inu njira ya cipulumutso.

18 Ndipo anacita cotero masiku ambiri. Koma Paulo anabvutika mtima ndithu, naceuka, nati kwa mzimuwo, Ndikulamulira iwe m'dzina la Yesu Kristu, turuka mwa iye. Ndipo unaturuka nthawi yomweyo.

19 Koma pamene ambuye ace anaona kuti kulingalira kwa kupindula kwao kwatha, anagwira Paulo ndi Sila, nawakokera kunka nao kubwalo kwa akuru,

20 ndipo pamene adanka nao kwa oweruza, anati, Anthu awa abvuta kwambiri mudzi wathu, ndiwo Ayuda,

21 ndipo alalikira miyambo imene siiloleka ife kuilandira, kapena kuicita, ndife Aroma.

22 Ndipo linagumukira iwo khamulo; ndipo oweruza anawang'ambira maraya ao; nalamulira kuti awakwapule.

23 Pamene anawaonetsa mikwingwirima yambiri, anawaika m'ndende, nauza mdindo kuti awasunge bwino.

24 Pakumva iye kulamulira kotero anawaika m'cipinda ca m'kati, namangitsa mapazi ao m'zigologolo.

25 Koma ngati pakati pa usiku, Paulo ndi Sila analinkupemphera, nayimbira Mulungu nyimbo, ndipo a m'ndendemo analinkuwamva;

26 ndipo mwadzidzidzi panali cibvomezi cacikuru, cotero kuti maziko a ndende anagwedezeka: pomwepo pamakomo ponse panatseguka; ndi maunyolo a onse anamasuka.

27 Pamene anautsidwa kutulo mdindoyo, anaona kuti pa makomo a ndende panatseguka, ndipo anasolola lupanga lace, nati adziphe yekha, poyesa kuti am'ndende adathawa.

28 Koma Paulo anapfuula ndi mau akuru, nati, Usadzipweteka wekha; tonse tiri muno.

29 Ndipo mdindo anaitanitsa nyali, natumphira m'kati, alinkunthunthunrlra ndi mantha, nagwa pamaso pa Paulo ndi Sila,

30 nawaturutsira iwo kunja, nati, Ambuye, ndicitenji kuti ndipulumuke?

31 Ndipo iwo anati, Ukhulupirire Ambuye Yesu, ndipo udzapulumuka, iwe ndi apabanja ako.

32 Ndipo anamuuza iye mau a Ambuye, pamodzi ndi onse a pabanja pace.

33 Ndipo anawatenga ora lomwelo la usiku, natsuka mikwingwirima yao; nabatizidwa pomwepo, iye ndi a pabanja pace.

34 Ndipo anakwera nao kunka kunyumba kwace, nawakhazikira cakudya, nasangalala kwambiri, pamodzi ndi a pabanja pace, atakhulupirira Mulungu.

35 Kutaca, oweruza anatumiza akapitao, kuti, Mukamasule anthu aja.

36 Ndipo mdindo anafotokozera mauwo kwa Paulo, nati, Oweruza atumiza mau kunena kuti mumuke; tsopanotu turukani, mukani mumtendere.

37 Koma Paulo anati kwa iwo, Adatikwapula ire pamaso pa anthu, osamva mlandu wathu, ire amene tiri Aroma, natiika m'ndende; ndipo tsopano kodi afuna kutiturutsira ire m'tseri? Iai, ndithu; koma adze okha atiturutse.

38 Ndipo akapitao anafotokozera mauwo kwa oweruza; ndipo iwowo anaopa, pakumva kuti anali Aroma.

39 Ndipo anadza nawapembedza; ndipo pamene anawaturutsa, anawapempha kuti acoke pamudzi.

40 Ndipo anaturukam'ndendemo, nalowa m'nyumba ya Lidiya: ndipo pamene anaona abale, anawasangalatsa, namuka.

17

1 Pamene anapitirira pa Amfipoli, ndi Apoloniya, anafika ku Tesalonika, kumene kunali sunagoge wa Ayuda.

2 Ndipo Paulo, monga amacita, analowa kwa iwo; ndipo masabata atatu ananena ndi iwo za m'malembo, natanthauzira,

3 natsimikiza, kuti kunayenera Kristu kumva zowawa, ndi kuuka kwa akufa; ndiponso kuti Yesu yemweyo, amene ndikulalikirani inu, ndiye Kristu.

4 Ndipo ena a iwo anakopedwa, nadziphatika kwa Paulo ndi Sila; ndi Ahelene akupembedza aunyinji ndithu, ndi akazi akuru osati owerengeka.

5 Koma Ayuda anadukidwa mtima, natenga anthu ena oipa acabe a pabwalo, nasonkhanitsa khamu la anthu, nacititsa phokoso m'mudzi; ndipo anagumukira ku nyumba ya Yasoni, nafuna kuwaturutsira kwa anthu.

6 Pamene sanawapeza anakokera Yasoni ndi abale ena pamaso pa akuru a mudzi, napfuula kuti, Omwe aja asanduliza dziko lokhalamo anthu, afika kunonso;

7 amene Yasoni walandira; ndipo onsewo acita zokana malamulo a Kaisara; nanena kuti pali mfumu yina, Yesu.

8 Ndipo anabvuta anthu, ndi akuru a mudzi, pamene anamva zimenezi.

9 Ndipo pamene analandira cikole kwa Yasoni ndi enawo, anawamasula.

10 Pomwepo abale anatumiza Paulo ndi Sila usiku kunka ku Bereya; pamene iwo anafika komweko analowa m'sunagoge wa Ayuda.

11 Amenewa anali mfulu koposa a m'Tesalonika, popeza analandira mau ndi kufunitsa kwa mtima wonse, nasanthula m'malembo masiku onse, ngati zinthu zinali zotero.

12 Ndipo ambiri a iwo anakhulupira; ndi akazi a Cihelene omveka, ndi amuna, osati owerengeka.

13 Koma pamene Ayuda a ku Tesalonika anazindikira kuti mau a Mulungu analalikidwa ndi Paulo ku Bereyanso, anadza komwekonso, nautsa, nabvuta makamu.

14 Pomwepo abale anaturutsa Paulo amuke kufikira kunyanja; koma Sila ndi Timoteo anakhalabe komweko.

15 Koma iwo amene anaperekeza Paulo anadza naye kufikira ku Atene; ndipo polandira iwo lamulo la kwa Sila ndi Timoteo kuti afulumire kudza kwa iye ndi cangu conse, anacoka.

16 Pamene Paulo analindira iwo pa Atene, anabvutidwa mtima pamene anaona mudzi wonse wadzala ndi mafano.

17 Cotero tsono anatsutsana ndi Ayuda ndi akupembedza m'sunagoge, ndi m'bwalo la malonda masiku onse ndi iwo amene anakomana nao.

18 Ndipo akukonda nzeru ena a Epikureya ndi a Stoiki anatengana naye. Ena anati, ici ciani afuna kunena wobwetuka uyu? Ndipo ena, Anga wolalikira ziwanda zacilendo, cifukwa analalikira Yesu ndi kuuka kwa akufa.

19 Ndipo anamgwira, nanka naye ku Areopagi, nati, Kodi tingathe kudziwa ciphunzitso ici catsopano ucinena iwe?

20 Pakuti ufika nazo ku makutu athu zacilendo: tifuna tsono kudziwa, izi zitani?

21 (Koma Aatene onse ndi alendo akukhalamo anakhalitsa nthawi zao, osacita kanthu kena koma kunena kapena kumva catsopano.)

22 Ndipo anaimirira Paulo pakati pa Areopagi nati, Amuna inu a Atene, m'zinthu zonse ndiona kuti muli akupembedzetsa.

23 Pakuti popita, ndi kuona zinthu zimene muzipembedza, ndipezanso guwa la nsembe lolembedwa potere, KWA MULUNGU WOSADZIWIKA. Cimene mueipembedza osacidziwa, cimeneco ndicilalikira kwa inu.

24 Mulungu amene analenga dziko lapansi ndi zonse ziri momwemo, Iyeyo, ndiye mwini kumwamba ndi dziko lapansi, sakhala m'nyumba zakacisi zomangidwa ndi manja;

25 satumikidwa ndi manja a anthu, monga wosowa kanthu, popeza iye mwini apatsa zonse moyo ndi mpweya ndi zinthu zonse;

26 ndipo ndi mmodzi analenga mitundu yonse ya anthu, kuti akhale ponse pa nkhope ya dziko lapansi, atapangiratu nyengo zao, ndi malekezero a pokhala pao;

27 kuti afunefune Mulungu, kapena akamfufuze ndi kumpeza, ngakhale sakhala patari ndi yense wa ife;

28 pakuti mwa iye tikhala ndi moyo ndi kuyendayenda, ndi kupeza mkhalidwe wathu; monga enanso a akuyimba anu ati, Pakuti ifenso tiri mbadwa zace.

29 Popeza tsono tiri mbadwa za Mulungu, sitiyenera kulingalira kuti umulungu uli wofanafana ndi golidi, kapena siliva, kapena mwala, woloca ndi luso ndi zolingalira za anthu.

30 Nthawi za kusadziwako tsono Mulungu analekerera; koma tsopanotu alinkulamulira anthu onse ponse ponse atembenuke mtima;

31 cifukwa anapangira tsiku limene adzaweruza dziko lokhalamo anthu m'cilungamo, ndi munthu amene anamuikiratu; napatsa anthu onse citsimikizo, pamene anamuukitsa iye kwa akufa.

32 Ndipo pamene anamva za kuuka kwa akufa ena anaseka pwepwete; koma ena anati, Tidzakumvanso za cimeneci.

33 Conco Paulo anaturuka pakati pao.

34 Koma ena anadziphatika kwa iye, nakhulupira; mwa iwonso munali Dionisiyo Mareopagi, ndi mkazi dzina lace Damarisi, ndi ena pamodzi nao.

18

1 Zitapita izi anacoka ku Atene, nadza ku Korinto.

2 Ndipo anapeza Myuda wina dzina lace Akula, pfuko lace la ku Ponto, atacoka catsopano ku Italiya, pamodzi ndi mkazi wace Priskila, cifukwa Klaudiyo analamulira Ayuda onse acoke m'Roma; ndipo Pauloanadza kwa iwo:

3 ndipo popeza anali wa nchito imodzimodzi, anakhala nao, ndipo iwowa anagwira nchito; pakuti nchito yao inali yakusoka mahema.

4 Ndipo anafotokozera m'sunagogemasabata onse, nakopa Ayuda ndi Ahelene.

5 Koma pamene Sila ndi Timoteo anadza potsika ku Makedoniya, Paulo anapsinjidwa ndi mau, nacitira umboni kwa Ayuda kuti Yesu ndiye Kristu.

6 Koma pamene iwo anamkana, nacita mwano, anakutumula maraya ace, nati kwa iwo, Mwazi wanu ukhale pa mitu yanu; ine ndiribe kanthu; kuyambira tsopano ndinka kwa amitundu.

7 Ndipo anacoka kumeneko, nalowa m'nyumba ya munthu, dzina lace Tito Yusto, amene anapembedza Mulungu, nyumba yace inayandikizana ndi sunagoge.

8 Ndipo Krispo, mkuru wasunagoge, anakhulupirira Ambuye, ndi apabanja ace onse; ndipo Akorinto ambiri anamva, nakhulupira, nabatizidwa.

9 Ndipo Ambuye anati kwa Paulo usiku m'masomphenya, Usaope, koma nena, usakhale cete;

10 cifukwa Ine ndiri pamodzi ndi iwe, ndipo palibe munthu adzautsana ndi iwe kuti akuipse; cifukwa ndiri nao anthu ambiri m'mudzi muno.

11 Ndipo anakhala komwe caka cimodzi kudza miyezi isanu ndi umodzi; naphunzitsamau a Mulungu mwa iwo.

12 Tsono pamene Galiyo anali ciwanga ca Akaya, Ayuda ndi mtima umodzi anamuukira Paulo, nanka naye ku mpando wa ciweruziro,

13 kuti, Uyu akopa anthu apembedze Mulungu pokana cilamulo.

14 Koma pamene Paulo anati atsegule pakamwa pace, Galiyo anati kwa Ayuda, Ukadakhala mlandu wa cosalungama, kapena dumbo loipa, Ayuda inu, mwenzi nditakumverani inu;

15 koma akakhala mafunso a mau ndi maina ndi cilamulo canu; muyang'ane inu nokha; sindifuna kuweruza zimenezi.

16 Ndipo anawapitikitsa pa mpando wa ciweruziro.

17 Ndipo anamgwira Sostene, mkuru wa sunagoge, nampanda ku mpando wa ciweruziro. Ndipo Galiyo sanasamalira zimenezi.

18 Paulo atakhala cikhalire masiku ambiri, anatsazika abale, nacoka pamenepo, napita m'ngalawa ku Suriya, pamodzi naye Priskila ndi Akula; popeza anameta mutu wace m'Kenkreya; pakuti adawinda.

19 Ndipo iwo anafika ku Efeso, ndipo iye analekana nao pamenepo: koma iye yekha analowa m'sunagoge, natsutsana ndi Ayuda.

20 Pamene iwo anamfunsa iye kuti akhale nthawi yina yoenjezerapo, sanabvomereza;

21 koma anawatsazika, nati, Akafuna Mulungu, ndidzabwera kwa inu; ndipo anacoka ku Efeso m'ngalawa.

22 Ndipo pamene anakoceza pa Kaisareya, anakwera nalankhulana nao Mpingo, natsikira ku Antiokeya.

23 Atakhala kumeneko nthawi, anacoka, napita pa dziko la Galatiya ndi Frugiya m'dziko m'dziko, nakhazikitsaakuphunzira onse.

24 Ndipo anafika ku Efeso Myuda wina dzina lace Apolo, pfuko lace la ku Alesandreya, munthu wolankhula mwanzeru; ndipo anali wamphamvu m'malembo.

25 Iyeyo aoaphunzitsidwa m'njira ya Ambuye; pokhala nao mzimu wacangu, ananena ndi kuphunzitsa mosamalira zinthu za Yesu, ndiye wodziwa ubatizo wa Yohane wokha;

26 ndipo iye anayamba kulankhula molimba mtima m'sunagoge, koma pamene anamumva iye Priskila ndi Akula, anamtenga, namfotokozera njira ya Mulungu mosamalitsa.

27 Ndipo pamene iye anafuna kuoloka kunka ku Akaya, abale anamfulumiza, ndi kulembera akalata kwa akuphunzira kuti amlandire: ndipo pamene anafika, iye anathangata ndithu iwo akukhulupira mwa cisomo;

28 pakuti ndi mphamvu anatsutsa Ayuda, pamaso pa anthu, nasonyeza mwa malembo kuti Yesu ndiye Kristu.

19

1 Ndipo panali, pamene Apolo anali ku Korinto, Paulo anapita pa maiko a pamtunda, nafika ku Efeso, napeza akuphunzira ena;

2 ndipo anati kwa iwo, Kodi munalandira Mzimu Woyera pamene munakhulupira? Ndipo anati, lai, sitinamva konsekuti Mzimu Woyera waperekedwa.

3 Ndipo anati, Nanga mwabatizidwa m'ciani? Ndipo anai, Mu ubatizo wa Yohane.

4 Ndipo anati Paulo, Yohane anabatiza ndi ubatizo wa kutembenuka mtima, nati kwa anthu, kuti amkhulupirire iye amene adzadza pambuyo pace, ndiye Yesu.

5 Pamene anamva ici, anabatizidwa m'dzina la Ambuye Yesu.

6 Ndipo pamene Paulo anaika manja ace pa iwo, Mzimu Woyera anadza pa iwo; ndipo analankhula ndi malilime, nanenera.

7 Onsewo anali ngati amuna khumi ndi awiri.

8 Ndipo iye analowa m'sunagoge, nanena molimba mtima, miyezi itatu, natsutsana ndi kukopa kunena za Ufumu wa Mulungu.

9 Koma pamene ena anaumitsa mtima ndi kusamvera, nanenera zoipa Njirayo pamaso pa anthu, anawacokera, napatutsa akuphunzira, nafotokozera masiku onse m'sukulu ya Turano.

10 Ndipo anacita comweco zaka ziwiri; kotero kuti onseakukhala m'Asiya anamva mau a Ambuye, Ayuda ndi Ahelene.

11 Ndipo Mulungu anacita zamphamvu za pa zokha ndi manja a Paulo;

12 kotero kuti anamuka nazo kwa odwala nsaru zopukutira ndi za panchito, zocokera pathupi pace, ndipo nthenda zinawacokera, ndi mizimu yoipa inaturuka.

13 Koma Ayuda enanso oyendayenda, oturutsa ziwanda, anadziyesa kuchula pa iwo amene anali ndi mizimu yoipa dzina la Ambuye Yesu, kuti, Ndikulumbirirani pa Yesu amene amlalika Paulo.

14 Ndipo panali ana amuna asanu ndi awiri a Skeva, Myuda, mkuru wa ansembe amene anacita ici.

15 Ndipo unayankha mzimu woipa, nuti kwa iwo, Yesu ndimzindikira, ndi Paulo ndimdziwa, koma inu ndinu ayani?

16 Ndipo munthu, mwa iye amene munali mzimu woipa, anawalumphira nawaposa, nawalaka onse awiriwo, kotero kuti anathawa m'nyumba amarisece ndi olasidwa.

17 Zimenezo zidamveka kwa onse, Ayuda ndi Ahelene, amene anakhala ku Efeso; ndipo mantha anagwera onsewo, ndipo dzina la Yesu Iinakuzika.

18 Ndipo ambiri a iwo akukhulipirawo anadza, nabvomereza, nafotokoza macitidwe ao.

19 Ndipo ambiri a iwo akucita zamatsenga anasonkhanitsa mabuku ao, nawatentha pamaso pa onse; ndipo anawerenga mtengo wace, napeza ndalama zasiliva zikwi makumi asanu.

20 Cotero mau a Ambuye anacuruka mwamphamvu nalakika.

21 Ndipo zitatha izi, Paulo anatsimikiza mu mzimu wace, atapita pa Makedoniya ndi Akaya, kunka ku Yerusalemu, kuti, Nditamuka komweko ndiyenera kuonanso ku Roma.

22 Pamene anatuma ku Makedoniya awiri a iwo anamtumikira, Timoteo ndi Erasto, iye mwini anakhalabe nthawi m'Asiya.

23 Nthawi yomweyo kunali phokoso lambiri kunena za Njirayo.

24 Pakuti munthu wina dzina lace Demetriyo wosula siliva, amene anapanga tiakacisi tasiliva ta Artemi, anaonetsera amisiri phindu lambiri;

25 amenewo iye anawasonkhanitsa pamodzi ndi amisiri a nchito yomweyo, nati, Amuna inu, mudziwa kuti ndi malonda awa ife tipeza cuma cathu.

26 Ndipo muona ndi kumva, kuti si pa Efeso pokha, koma monga pa Asiya ponse, Paulo uyu akopa ndi kutembenutsa anthu ambiri, ndi kuti, Si milungu iyi imene ipangidwa ndi manja:

27 ndipo tiopa ife kuti nchito yathuyi idzayamba kunyonyosoka; komanso kuti kacisi wa mlungu wamkazi Artemi adzayamba kuyesedwa wacabe; ndiponso kuti iye adzayamba kutsitsidwa ku ukulu wace, iye amene a m'Asiya onse, ndi onse a m'dziko lokhalamo anthu, ampembedza.

28 Ndipo pamene anamva, anadzala ndi mkwiyo, napfuula, nati, Wamkuru ndi Artemi wa ku Efeso,

29 Ndipo m'mudzi monse munacita piringu-piringu, nathamangira onse pamodzi ku bwalo losewera, atagwira Gayo ndi Aristarko, anthu a ku Makedoniya, alendo anzace a Paulo.

30 Ndipo pamene Paulo anafuna kulowa kwa anthu, akuphunzira ace sanamloleza.

31 Ndipo akulu ena a Asiyanso, popeza anali abwenzi ace, anatumiza mau kwa iye, nampempha asadziponye ku bwalo lakusewera.

32 Ndipo ena anapfuula kanthu kena, ena kanthu kena; pakuti msonkhanowo unasokonezeka; ndipo unyinji sunadziwa cifukwa cace ca kusonkhana.

33 Ndipo anaturutsa Alesandro m'khamumo, kumturutsa iye Ayuda. Ndipo Alesandro anatambasula dzanja, nafuna kudzikanira kwa anthu adasonkhanawo.

34 Koma pozindikira kuti ali Myuda, kunali mau amodzi a kwa onse akupfuula monga maora awiri, Wamkuru ndi Artemi wa Aefeso.

35 Ndipo pamene mlembi adatontholetsa khamulo, anati, Amuna a Efeso inu, munthuyu ndani wosadziwa kuti mudzi wa Aefeso ndiwo wosungira kacisi wa Artemi wamkuru, ndi fano Iidacokera kwa Zeu?

36 Popeza tsono izi sizikanika, muyenera inu kukhala cete, ndi kusacita kanthu kaliuma.

37 Pakuti mwatenga anthu awa, osakhala olanda za m'kacisi, kapena ocitira mulungu wathu mwano.

38 Ngati tsono Demetriyo ndi amisiri okhala naye, ali ndi mlandu ndi munthu, mabwalo a mirandu alipo, ndi ziwanga ziripo; anenezane.

39 Koma ngati mufuna kanthu ka zinthu zina, kadzakonzeka m'msonkhano wolamulidwa.

40 Pakutinso palipo potiopsya kuti adzatineneza za cipolowe ca lero; popeza palibe cifukwa ca kufotokozera za cipiringu cimene.

41 Ndipo pamene ananena izi, anamasula msonkhano.

20

1 Ndipo litaleka phokoso, Paulo anaitana ophunzirawo, ndipo m'mene anawacenjeza, analawirana nao, naturuka kunka ku Makedoniya.

2 Ndipo m'mene atapitapita m'mbali zijazo, nawacenjeza, anadza ku Helene.

3 Ndipo m'mene adakhalako miyezi itatu, ndipo a atampangira ciwembu Ayuda, pori iye apite ndi ngalawa ku Suriya, anatsimikiza mtima abwerere popyola Makedoniya.

4 Ndipo anamperekeza kufikira ku Asiya Sopatro mwana wa Puro, wa ku Bereya; ndipo Atesalonika, Aristarko ndi Sekundo; ndi Gayo wa ku Derbe, ndi Timoteo; ndi a ku Asiya, Tukiko ndi Trofimo.

5 Koma iwowa adatitsogolera, natilinda ku Trowa.

6 Ndipo tinapita m'ngalawa kucokera ku Filipi, atapita masiku a mkate wopanda cotupitsa, ndipo popita masiku asanu tinawapeza ku Trowa; pamenepo tinatsotsa masiku asanu ndi awiri.

7 Ndipo tsiku loyamba la sabata, posonkhana ife kunyema mkate, Paulo anawafotokozera mau, popeza anati acoke m'mawa mwace; ndipo ananena cinenere kufikira pakati pa usiku.

8 Ndipo munali nyali zambiri m'cipinda ca pamwamba m'mene tinasonkhanamo.

9 Ndipo mnyamata dzina lace Utiko anakhala pazenera, wogwidwa nato tulo tatikuru; ndipo pakukhala cifotokozere Paulo, ndipo pogwidwa nato tulo, anagwa posanja paciwiri, ndipo anamtola wakufa.

10 Ndipo potsikirako Paulo, anamgwera namfungatira, nati, Musacite phokoso, pakuti moyo wace ulipo.

11 Ndipo m'mene adakwera, nanyema mkate, nadya, nakamba nao nthawi, kufikira kuca, anacokapo,

12 Ndipo anadza naye mnyamata ali wamoyo, natonthozedwa kwakukuru.

13 Koma ife tinatsogolera kunka kungalawa, ndipo tinapita ku Aso, pamenepo tinati timlandire Paulo; pakuti anatipangira comweco, koma anati ayenda pamtunda yekha.

14 Ndipo pamene anakomana ndi ife ku Aso, tinamlandira, ndipo tinafika ku Mitilene.

15 Ndipo m'mene tidacokerapo, m'mawa mwace tinafika pandunjipa Kiyo; ndi m'mawa mwace tinangokoceza ku Samo, ndi m'mawa mwace tinafika ku Mileto.

16 Pakuti Paulo adatsimikiza mtima apitirire pa Efeso, angataye nthawi m'Asiya; pakuti anafulumira, ngati kutheka, akhale ku Yerusalemu tsiku la Pentekoste.

17 Ndipo pokhala ku Mileto anatuma ku Efeso, naitana akulu a Mpingo.

18 Ndipo pamene anafika kuli iye, anati kwa iwo, Mudziwa inu kuyambira tsiku loyamba ndinafika ku Asiya, makhalidwe anga pamodzi ndi inu nthawi yonse,

19 wotumikira Ambuye ndi kudzicepetsa konse ndi misozi, ndi mayesero anandigwera ndi ziwembu za Ayuda;

20 kuti sindinakubisirani zinthu zopindulira, osazilalikira kwa inu, ndi kukuphunzitsani inu pabwalo ndi m'nyumba m'nyumba,

21 ndi kucitira umboni Ayuda ndi Ahelene wa kutembenuza mtima kulinga kwa Mulungu, ndi cikhulupiriro colinga kwa Ambuye wathu Yesu Kristu.

22 Ndipo, taonani, ndipita ku Yerusalemu womangidwa mumzimu, wosadziwa zimene zidza'ndigwera ine kumeneko;

23 koma kuti Mzimu Woyera andicitira umboni m'midzi yonse, ndi kunena kuti nsinga ndi zisautso zindilindira.

24 Komatu sindiuyesa kanthu moyo, wanga, kuti uli wa mtengo wace kwa ine ndekha; kotero kuti ndikatsirize njira yanga, ndi utumiki ndinaulandira kwa Ambuye Yesu, kucitira umboni Uthenga Wabwino wa cisomo ca Mulungu.

25 Ndipo tsopano, taonani, ndidziwa ine kuti inu nonse amene ndinapitapita mwa inu kulalikira ufumuwo, simudzaonanso nkhope yanga.

26 Cifukwa cace ndikucitirani umboni lero lomwe, kuti ndiribe kanthu ndi mwazi wa anthu onse.

27 Pakuti sindinakubisirani pakukulalikirani uphungu wonse wa Mulungu.

28 Tadzicenjerani nokha, ndi gulu lonse, pamenepo Mzimu Woyera anakuikani oyang'anira, kuti muwete Eklesia wa Mulungu, umene anaugula ndi mwazi wa iye yekha.

29 Ndidziwa ine kuti, nditacoka ine, adzalowa mimbulu yosautsa, yosalekerera gululo;

30 ndipo mwa inu nokha adzauka anthu, olankhula zokhotakhota, kupatutsa ophunzira awatsate.

31 Cifukwa cace dikirani, nimukumbukile kuti zaka zitatu sindinaleka usiku ndi usana kucenjeza yense wa inu ndi misozi.

32 Ndipo tsopano ndikuikizani kwa Mulungu, ndi kwa mau a cisomo cace, cimene ciri ndi mphamvu yakumangirira ndi kupatsa inu colowa mwa onse oyeretsedwa.

33 Sindinasirira siliva, kapena golidi, kapena cobvala ca munthu ali yense.

34 Mudziwa inu nokha kuti manja anga awa anatumikira zosowa zanga, ndi za iwo akukhala ndi ine.

35 M'zinthu zonse ndinakupatsani citsanzo, cakuti pogwiritsa nchito, koteromuyenerakuthandiza ofoka ndi kukumbuka mau a Ambuye Yesu, kuti anati yekha, Kupatsa kutidalitsa koposa kulandira.

36 Ndipo m'mene ananena izi, anagwada pansi, napemphera ndi iwo onse.

37 Ndipo onsewa analira kwambiri, namkupatira Paulo pakhosi pace, nampsompsona,

38 nalira makamaka cifukwa ca mau adanenawa, kuti sadzaonanso nkhope yace. Ndipo anamperekeza iye kungalawa.

21

1 Ndipo kunali, titalekana nao ndi kukankha ngalawa, tinadza molunjika ku Ko, ndi m'mawa mwace ku Rode, ndipo pocokerapo ku Patara;

2 ndipo m'mene tinapeza ngalawa Yakuoloka kunka ku Foinike, tinalowamo, ndi kupita nayo.

3 Ndipo pamene tinafika popenyana ndi Kupro, tinacisiya kulamanzere, ntinapita ku Suriya; ndipo tinakoceza ku Turo; pakuti pamenepo ngalawainafuna kutula akatundu ace.

4 Ndipo m'mene tinapeza ophunzira, tinakhalako masikuasanu ndi awiri; ndipo iwowa ananena ndi Paulo mwa Mzimu, kuti asakwere ku Yerusalemu.

5 Ndipo kunali pamene tidatsiriza masikuwa, tidacoka ndi kunka ulendo wathu; ndipo iwo onse, akazi ndi ana anatiperekeza kufikira kuturuka m'mudzi; ndipo pogwadira pa mcenga wa kunyanja, tinapemphera,

6 ndi kulawirana; ndipo tinalowa m'ngalawa, koma iwo anabwera kwao.

7 Ndipo ife titatsiriza ulendo wathu wocokera ku Turo, tinafika ku Ptolemayi; ndipo m'mene tidalankhula abale, tinakhala nao tsiku limodzi.

8 Ndipo m'mawa mwace tinacoka, ntinafika ku Kaisareya, ndipo m'mene tinalowa m'nyumba ya Filipo mlaliki, mmodzi wa asanu ndi awiri aja, tinakhala naye.

9 Ndipo munthuyu anali nao ana akazi anai, anamwali, amene ananenera.

10 Ndipo pokhalapo masiku ambiri, anatsika ku Yudeya mneneri, dzina lace Agabo.

11 Ndipo anadza kwa ife natenga lamba la Paulo, nadzimanga yekha manja ndi mapazi, nati, Atero Mzimu Woyera, Munthu mwini lamba ili, adzammanga kotero Ayuda a m'Yerusalemu, nadzampereka m'manja a amitundu.

12 Koma pamene tinamva izi tinamdandaulira ife ndi iwo a komweko, asakwere iye kunka ku Yerusalemu.

13 Pamenepo Paulo anayankha, Mucitanji, polira ndi kundiswera mtima? pakuti ndakonzeka Ine si kumangidwa kokha, komatunso kufera ku Yerusalemu cifukwa ca dzina la Ambuye Yesu.

14 Ndipo pokana iye kukopeka, tinaleka, ndi kuti, Kufuna kwa Ambuye kucitidwe.

15 Ndipo atapita masiku awa tinakonza akatundu athu, ntikwera ku Yerusalemu.

16 Ndipo anamuka nafenso ena a ophunzira a ku Kaisareya, natenganso wina Mnaso wa ku Kupro, wophunzira wakale, amene adzaticereza.

17 Ndipo pofika ife ku Yerusalemu, abale anatilandira mokondwera.

18 Ndipo m'mawa mwace Paulo analowa nafe kwa Yakobo; ndi akulu onse anali pomwepo.

19 Ndipo atawalankhula iwo, anawafotokozera cimodzi cimodzi zimene Mulungu anacita kwa amitundu mwa utumiki wace.

20 Ndipo pamene anazimva, analemekeza Mulungu; nati kwa iye, Uona, mbale, kuti ambirimbiri mwa Ayuda akhulupira; ndipo ali naco cangu onsewa, ca pa cilamulo;

21 ndipo anamva za iwe, kuti uphunzitsa Ayuda onse a ku amitundu apatukane naye Mose, ndi kuti asadule ana ao, kapena asayende monga mwa miyambo.

22 Nciani tsono? adzamva ndithu kuti wafika.

23 Cifukwa cace ucite ici tikuuza iwe; tiri nao amuna anai amene anawinda;

24 amenewa uwatenge nudziyeretse nao pamodzi, nuwalipirire, kati amete mutu; ndipo adzadziwa onse kuti zomveka za iwe nzacabe, koma kuti iwe wekhaoso uyenda molunjika, nusunga cilamulo.

25 Kama kunena za amitundu adakhulupirawo, tinalembera ndi kulamulira kuti asale zoperekedwa kwa mafano, ndi mwazi, ndi zopotola, ndi dama.

26 Pamenepo Paulo anatenga anthuwo, ndipo m'mawa mwace m'mene anadziyeretsa nao pamodzi, analowa m'Kacisi, nauza cimarizidwe ca masiku a kuyeretsa, kufikira adawaperekera iwo onse mtulo.

27 Ndipo pamene masiku asanu, ndi awiri anati amarizidwe, Ayuda a ku Asiya pomuona iye m'Kacisi, anautsa khamu lonse la anthu, namgwira,

28 napfuula, Amuna a Israyeli, tithandizeni; ameneyu ndi munthu uja anaphunzitsa onse ponsepo ponenera anthu, ndi cilamulo, ndi malo ano; ndiponso anatenga Ahelene nalowa nao m'Kacisi, nadetsa malo ana oyera.

29 Pakuti adaona Trofimo wa ku Efeso kale pamodzi ndi iye mumzinda; ameneyo anayesa kuti Paulo anamtenga nalowa naye kuKacisi.

30 Ndipo mudzi wonse unasokonezeka, ndipo anthu anathamangira pamodzi; nagwira Paulo namkoka kumturutsa m'Kacisi; ndipo pomwepo pamakomo panatsekedwa.

31 Ndipo m'mene anafuna kumupha iye, wina anamuuza kapitao wamkuru wa gululo kuti m'Yerusalemumonse muli pinngu-piringu,

32 Ndipo posacedwa iye anatenga asilikari ndi akenturiyo, nathamanga, nawatsikira; ndipo iwowa, pakuona kapitao wamkuru ndi asilikari, analeka kumpanda Paulo.

33 Pamenepo poyandikira kapitao wamkuru anamgwira iye, nalamulira ammange ndi maunyolo awir; ndipo anafunsira, ndiye yani, ndipo anacita ciani?

34 Koma wina anapfuula kena, wina kena, m'khamumo; ndipo m'mene sanathe kudziwa zoona cifukwa ca phokosolo analamulira amuke naye kulinga.

35 Ndipo pamene anafika pamakwerero, kudatero kuti anamsenza asilikari cifukwa ca kulimbalimba kwa khamulo;

36 pakuti unyinji wa anthu unatsata, nupfuula, Mcotse iye.

37 Ndipo poti alowe naye m'linga, Paulo ananena kwa kapitao wamkuru, Mundilole ndikuuzeni kanthu? Ndipo anati, Kodi udziwa Cihelene?

38 Si ndiwe M-aigupto uja kodi, unacita mipanduko kale lija, ndi kutsogolera ambanda aja zikwi zinai kucipululu?

39 Koma Paulo anati, Ine ndine munthu Myuda, wa ku Tariso wa m'Kilikiya, mfulu ya mudzi womveka; ndipo ndikupemphani mundilole ndilankhule ndi anthu.

40 Ndipo m'mene adamlola, Paulo anaimirira pamakwerero, natambalitsira anthu dzanja; ndipo pokhala cete onse, analankhula nao m'cinenedwe ca Cihebri, nanena.

22

1 Amuna, abale, ndi atate, mverani codzikanira canga tsopano, ca kwa inu.

2 Ndipo pakumva kuti analankhula nao m'cinenedwe ca Cihebri, anaposa kukhala cete; ndipo anati:

3 ine ndine munthu Myuda, wobadwa m'Tariso wa Kilikiya, koma ndaleredwa m'mzinda muno, pa mapazi a Gamaliyeli, wolangizidwa monga mwa citsatidwe ceni ceni ca cilamulo ca makolo athu, ndipo ndinali wacangu, colinga kwa Mulungu, monga muli inu nonse lero;

4 ndipo ndinalondalonda Njira iyi kufikira imfa, ndi kumanga ndi kupereka kundende amuna ndi akazi.

5 Monganso mkulu wa ansembe andicitira umboni, ndi bwalo lonse la akuru; kwa iwo amenenso ndinalandira akalata kunka nao kwa abale, ndipo ndinapita ku Damasiko, kuti ndikatenge iwonso akukhala kumeneko kudza nao omangidwa ku Yerusalemu, kuti alangidwe.

6 Ndipo kunali, pakupita ine ndi kuyandikira ku Damasiko, monga usana, mwadzidzidzi kunandiwalira pondizungulira ine kuunika kwakukuru kocokera kumwamba.

7 Ndipo ndinagwapansitu, ndipondinamva mau akunena nane, Saulo, Saulo, undilonda-londeranii Ine?

8 Ndipo ndinayankha, Ndinu yani Mbuye? Ndipo anati kwa Ine, Ndine Yesu wa ku Nazarete, amene umlondalonda.

9 Ndipo iwo akukhala nane anaonadi kuunika, koma sanamva mau akulankhula nane.

10 Ndipo ndinati, ndidzacita ciani, Ambuye? Ndipo Ambuye anati kwa ine, Taukavpita ku Damasiko; kumeneko adzakufotokozera zonse zoikika kwa iwe uzicite.

11 Ndipo popeza sindinapenya, cifukwa ca ulemerero wa kuunikako, anandigwira dzanja iwo amene anali ndi ine, ndipo ndinafika ku Damasiko.

12 Ndipo munthu dzina lace Hananiya, ndiye munthu wopembedza monga mwa cilamulo, amene amcitira umboni wabwino Ayuda onse akukhalako,

13 anadza kwa ine, ndipo poimirirapo anati kwa ine, Saulo, mbale, penyanso. Ndipo ine, ora lomweli ndinampenya.

14 Ndipo anati, Mulungu wa makolo athu anakusankhiratu udziwe cifuniro cace, nuone Wolungamayo, numve mau oturuka m'kamwa mwace.

15 Ndipo udzamkhalira iye mboni kwa anthu onse, za izo udaziona ndi kuzimva.

16 Ndipo tsopano ucedweranji? Tauka, nubatizidwe ndi kusamba kucotsa macimo ako, nuitane pa dzina lace.

17 Ndipo kunali, nditabwera ku Yerusalemu ndinalikupemphera m'Kacisi, ndinacita ngati kukomoka,

18 ndipo ndinamuona iye, nanena nane, Fulumira, turuka msanga m'Yerusalemu; popeza sadzalandira umboni wako wakunena za Ine.

19 Ndipo ndinati ine, Ambuye, adziwa iwo okha kuti ndinali kuika m'ndende ndi kuwapanda m'masunagoge onse iwo akukhulupirira Inu;

20 ndipo pamene anakhetsa mwazi wa Stefano mboni yanu, ine ndemwe ndinalikuimirirako, ndi kubvomerezana nao, ndi kusunga Zoobvala za iwo amene anamupha iye.

21 Ndipo anati kwa ine, Pita; cifukwa Ine ndidzakutuma iwe kunka kutali kwa amitundu.

22 Ndipo adamumva kufikira mau awa; ndipo anakweza mau ao nanena, Acoke pa dziko lapansi munthu wotere; pakuti sayenera iye kukhala ndi moyo.

23 Ndipo pakupfuula iwo, ndi kutaya zobvala zao, ndi kuwaza pfumbi mumlengalenga,

24 kapitao wamkuru analamulira kuti amtenge iye kulowa naye kulinga, nati amfunsefunse ndi kumkwapula, kuti adziwe cifukwa cace nciani kuti ampfuulira comweco.

25 Ndipo m'mene anammanga iye ndi nsingazo, Paulo anati kwa kenturiyo wakuimirirako, Kodinkuloleka kwa inu kukwapula munthu Mroma, mlandu wace wosamveka?

26 Ndipo pakumva ici kenturiyoyo, ananka kwa kapitao wamkuru, namuuza, nanena, Nciani ici uti ucite? pakuti munthuyo ndiye Mroma.

27 Ndipo kapitao wamkuruyo anadza, nati kwa iye, Ndiuze, iwe ndiwe Mroma kodi? Ndipo anati, Inde.

28 Ndipo kapitao wamkuru anayankha, Ine ndalandira ufulu umene ndi kuperekapo mtengo wace waukuru. Ndipo Paulo anati, Koma ine ndabadwa Mroma.

29 Pamenepo ndipo iwo amene anati amfunsefunse, anamsiya; ndipo kapitao wamkurunso anaopa, pozindikira kuti ndiye Mroma, ndiponso popeza adammanga iye.

30 Koma m'mawa mwace pofuna kuzindikira cifukwa cace ceni ceni cakuti anamnenera Ayuda, anammasula iye, nalamulira asonkhane ansembe akulu, ndi bwalo lonse la akulu, ndipo anatsika naye Paulo, namuika pamaso pao.

23

1 Ndipo Paulo, popenyetsetsa a m'bwalo la akuru anati, Amuna, abale, ndakhala ine pamaso pa Mulungu ndi cikumbu mtima cokoma conse kufikira lero lomwe.

2 Ndipo mkulu wa ansembe Hananiya analamulira akuimirirako ampande pakamwa pace.

3 Pamenepo Paulo anati kwa iye, Mulungu adzakupanda iwe, khoma loyeretsedwa iwe; ndipo kodi ukhala iwe wakundiweruza mlandu monga mwa cilamulo, ndipo ulamulira andipande ine posanga cilamulo?

4 Ndipo iwo akuimirirako anati, Ulalatira kodi mkulu wa ansembe wa Mulungu?

5 Ndipo Paulo anati, Sindinadziwa, abale, kuti ndiye mkulu wa ansembe; pakuti kwalembedwa, Usamnenera coipa mkulu wa anthu ako.

6 Koma pozindikira Paulo kuti ena ndi Asaduki, ndi ena Afarisi, anapfuula m'bwalomo, Amuna, abale, ine ndine Mfarisi, mwana wa Afarisi: andinenera mlandu wa ciyembekezo ndi kuuka kwa akufa.

7 Ndipo pamene adatero, kunakhala cilekano pakati pa Afarisi ndi Asaduki; ndipo osonkhanawo anagawikana.

8 Pakutitu Asaduki anena kuti kulibe kuuka kwa akufa, kapena mngelo, kapena mzimu; koma Afarisi abvomereza ponse pawiri.

9 Ndipo cidauka cipolowe cacikuru; ndipo alembi ena a kwa Afarisi anaimirira, natsutsana, nanena, Sitipeza coipa ciri conse mwa munthuyu; ndipo nanga bwanji ngati mzimu kapena mngelo: walankhula naye?

10 Ndipo pamene padauka cipolowe cacikuru, kapitao wamkuru anaopa kuti angamkadzule Paulo, ndipo analamulira asilikari atsike, namkwatule pakati pao, nadze naye kulowa naye m'linga,

11 Ndipo usiku wace Ambuye anaimirira pa iye, nati, Limbika mtima; pakuti monga wandicitira umboni ku Yerusalemu, koteronso uyenera kundicitira umboni ku Roma.

12 Ndipo kutaca, Ayuda anapangana ciwembu, nadzitemberera, ndi kunena kuti sadzadya kapena kumwa kanthu, kufikira atamupha Paulo;

13 ndipo iwo amene adacita cilumbiro ici anali oposa makumi anai.

14 Amenewo anadza kwa ansembe akulu ndi akulu, nati, Tadzitemberera nalo temberero kuti sitidzalawa kanthu kufikira titamupha Paulo.

15 Potero tsopano inu ndi bwalo la akuru muzindikiritse kapitao wamkuru kuti atsikenaye kwa inu, monga ngati mufuna kudziwitsitsa bwino za iye; koma tadzikonzeratu timuphe asanayandikire iye.

16 Koma mwana wa mlongo wace wa Paulo anamva za cifwamba cao, ndipo anadza nalowa m'linga, namfotokozera Paulo.

17 Ndipo Paulo anadziitanira kenturiyo wina, nati, Pita naye mnyamata uyu kwa kapitao wamkuru; pakuti ali nako kanthu kakumfotokozera iye.

18 Pamenepo ndipo anamtenga, napita naye kwa kapitao wamkuru, nati, Wam'nsingayo Paulo anandiitana, nandipempha ndidze naye mnyamata uyu kwa inu, ali nako kanthu kakulankhula ndi inu.

19 Ndipo kapitao wamkuru anamgwira dzanja, napita naye padera, namfunsa m'tseri, Ciani ici uli naco kundifotokozera?

20 Ndipo anati, Ayuda anapangana kuti akufunseni mutsike naye Paulo mawa ku bwalo la mirandu, monga ngati mufuna kufunsitsa za iye.

21 Pamenepo musakopedwe nao; pakuti amlalira iye oposa makumi anai a iwo amene anadzitemberera okha kud sadzadya kapena kumwa kufikira atamupha iye; ndipo akonzekeratu tsopano nayang'anira lonjezano lanu.

22 Pamenepo ndipo kapitao wamkuru anauza mnyamatayo apite, namlamulira kuti, Usauze munthu yense kuti wandizindikiritsa izi.

23 Ndipo anaitana akenturiyo awiri, nati, Mukonzeretu asilikari mazana awiri, apite kufikira Kaisareya, ndi apakavalo makumi asanu ndi awiri, ndi anthungo mazana awiri, acoke ora lacitatu la usiku;

24 ndiponso mukonzeretu nyama zobereka amkwezepo Paulo, nampereke wosungika kwa Felike kazembeyo.

25 Ndipo analembera kalata wakuti:

26 Klaudiyo Lusiya kwa kazembe womveketsa Felike, ndikulankhulani.

27 Munthu uyu anagwiridwa ndi Ayuda, ndipo akadaphedwa ndi iwo; pamenepo ndinafikako ine ndi asilikari, ndipo ndinamlanditsa pakumva kuti ndiye Mroma.

28 Ndipo pofuna kuzindikira cifukwa cakuti anamnenera iye, ndinatsikira naye ku bwalo la akuru ao.

29 Ndipo ndinapeza kuti adamnenera za mafunso a cilamulo cao; koma analibe kumnenera kanthu kakuyenera imfa kapena nsinga.

30 Ndipo m'mene anandidziwitsa kuti pali ciwembu ca pa munthuyu, pomwepo ndinamtumiza kwa inu; ndipo ndalamulira akumnenera akamnenere kwa inu.

31 Pamenepo ndipo asilikari, monga adawalamulira, anatenga Paulo, napita naye usiku ku Antipatri.

32 Koma m'mawa mwace anasiya apakavalo amperekeze, nabwera kulinga;

33 iwowo, m'mene anafika ku Kaisareya, anapereka kalata kwa kazembe, naperekanso Paulo kwa iye.

34 Ndipo m'mene adawerenga anafunsa acokera m'dziko liti; ndipo pozindikira kuti anali wa ku Kilikiya,

35 anati, Ndidzamva mlandu wako, pamene akukunenera afika. Ndipo analamulira kuti amdikire iye m'nyumba yamlandu ya Herode.

24

1 Ndipo atapita masiku asanu anatsika mkulu wa ansembe Hananiya pamodzi ndi akuru ena, ndi wogwira moyo dzina lace Tertulo; ndipo anafotokozera kazembeyo za kunenera Paulo.

2 Ndipo pamene adamuitana, Tertulo anayamba kumnenera ndi kunena. Popeza tiri nao mtendere wambiri mwa inu, ndipo mwa kuganiziratu kwanu muukonzera mtundu wathu zotiipsa,

3 tizilandira ndi ciyamiko conse, monsemo ndi ponsepo, Felike womveka inu.

4 Koma kuti ndingaonjeze kukulemetsani ndikupempha, ni mutimvere mwacidule ndi cifatso canu.

5 Pakuti tapeza munthuyu ali ngati mliri, ndi woutsa mapanduko kwa Ayuda onse m'dziko lonse lokhalamo anthu, ndi mtsogoleri wa mpanduko wa Anazarene;

6 amenenso anayesa kuipsa Kacisi; amene tamgwira;

7

8 kwa iye mudzakhoza kuzindikira pomfunsa nokha, za izi zonse timnenerazi.

9 Ndipo Ayudanso anabvomerezana naye, natsimikiza kuti izi zitero.

10 Ndipo pamene kazembe anamkodola kuti anene, Paulo anayankha, Podziwa ine kuti mwakhala woweruza wa mtundu uwu zaka zambiri, ndidzikanira mokondwera;

11 popeza mukhoza kuzindikira kuti apita masiku khumi ndi awiri okha cikwerere ine ku Yerusalemu kukalambira;

12 ndipo sanandipeza m'Kacisi wotsutsana ndi munthu, kapena kuutsa khamu la anthu, kapena m'sunagoge kapena m'mzinda.

13 Ndipo sangathe kukutsimikizirani zimene andinenera ine tsopano.

14 Koma ici ndibvomera kwa inu, kuti monga mwa Njira yonenedwa mpatuko, momwemo nditumikira Mulungu wa makolo athu, ndi kukhulupira zonse ziri monga mwa cilamulo, ndi zolembedwa mwa aneneri;

15 ndi kukhala naco ciyembekezo ca kwa Mulungu cimene iwo okhanso acilandira, kuti kudzakhala kuuka kwa olungama ndi osalungama.

16 M'menemonso ndidziyesera ndekha ndikhale naco nthawi zonse cikumbu mtima cosanditsutsa ca kwa Mulungu ndi kwa anthu.

17 Ndipo zitapita zaka zambiri ndinadza kutengera mtundu wanga zacifundo, ndi zopereka;

18 popereka izi anandipeza woyeretsedwa m'Kacisi, wopanda khamu la anthu, kapena phokoso; koma panali Ayuda ena a ku Asiya,

19 ndiwo mwenzi atakhala pano pamaso panu ndi kundinenera, ngati ali nako kanthu kotsutsa ine.

20 Kapena iwo amene ali kunowa anene anapeza cosalungama cotani, poimirira ine pamaso pa bwalo la akuru,

21 koma mau awa amodzi okha, amene ndinapfuula poimirira pakati pao, Kunena za kuuka kwa akufa ndiweruzidwa ndi inu lero lino.

22 Koma Felike anawalinditsa, popeza anadziwitsadi Njirayo, nati, Pamene Lusiya kapitao wamkuru akatsika ndidzazindikiritsa konse za kwa inu.

23 Ndipo analamulira kenturiyo amsunge iye, koma akhale nao ufulu, ndipo asaletse anthu ace kumtumikira.

24 Koma atapita masiku ena, anadza Felike ndi Drusila mkazi wace, ndiye Myuda, naitana Paulo, ndipo anamva iye za cikhulupiriro ca Kristu Yesu.

25 Ndipo m'mene anamfotokozera za cilungamo, ndi cidziletso, ndi ciweruziro cirinkudza, Felike anagwidwa ndi mantha, nayankha, Pita tsopano; ndipo ndikaona nthawi, ndidzakuitana iwe.

26 Anayembekezanso kuti Paulo adzampatsa ndalama; cifukwa cacenso anamuitana iye kawiri kawiri, nakamba naye.

27 Koma zitapita zaka ziwiri Porkiyo Festo analowa m'malo a Felike; ndipo Felike pofuna kukonda Ayuda anamsiya Paulo m'nsinga.

25

1 Pamenepo Festo m'mene analowa dziko lace, ndipo atapita masiku atatu, anakwera kunka ku Yerusalemu kucokera ku Kaisareya.

2 Ndipo ansembe akulu ndi akulu a Ayuda ananenera Paulo kwa iye; ndipo iwo anamdandaulira,

3 nampempha kuti mlandu wace wa Paulo uipe, kuti amuitane iye adze ku Yerusalemu; iwo amcitira cifwamba kuti amuphe panjira.

4 Pamenepo Festo anayankha, kuti Paulo asungike ku Kaisareya, ndi kuti iye mwini adzapitako posacedwa.

5 Cifukwa cace, ati, iwo amene akhoza mwa inu amuke nane potsikirako, ndipo ngati kuli kanthu kosayenera mwa munthuyo amnenere iye.

6 Ndipo m'mene adatsotsa mwa iwo masiku asanu ndi atatu kapena khumi okha anatsikiraku Kaisareya; ndipo m'mawa mwace anakhala pa mpando waciweruziro, nalamulira kuti atenge Paulo.

7 Ndipo m'mene anafika iye, Ayuda adatsikawo ku Yerusalemu anaimirira pomzinga iye, namnenera zifukwa zambiri ndi zazikuru, zimene sanakhoza kuzitsimikiza;

8 koma Paulo podzikanira ananena, Sindinacimwa kanthu kapena pacilamulo, kapena paKacisi, kapena pa Kaisara.

9 Kama Festo pofuna kuyesedwa wacisomo ndi Ayuda, anayankha kwa Paulo, nati, Kodi ufuna kukwera kunka ku Yerusalemu, ndi kuweruzidwa ndi ine pomwepo kunena za zinthu izi?

10 Koma Paulo anati, ndirikuimirira pa mpando waciweruziro wa Kaisara, pompano ndiyenera kuweruzidwa ine; Ayuda sindinawacitira-kanthu koipa, monga mudziwanso nokha bwino.

11 Pamenepo ngati ndiri wocita zoipa, ngati ndacita kanthu kakuyenera imfa, sindikana kufa; koma ngati zinthuzi awa andinenera nazo ziri zacabe, palibe mmodzi akhoza kundipereka kwa iwo. Nditurukira kwa Kaisara.

12 Pamenepo Festo, atakamba ndi aphungu ace, anayankha, Wanena, Ndirurukira kwa Kaisara; kwa Kaisara udzapita.

13 Ndipo atapita masiku ena, Agripa mfumuyo, ndi Bemike anafika ku Kaisareya, nalankhula Festo.

14 Ndipo atatsotsako masiku ambiri, Festo anafotokozera mfumuyo mlandu wace wa Paulo, nanena, Pali munthu adamsiya m'ndende Felike,

15 amene ansembe akulu ndi akulu a Ayuda anamnenera kwa ine, ndiri ku Yerusalemu, nandipempha ndiipitse mlandu wace.

16 Koma ndinawayankha, kuti macitidwe a Aroma satero, kupereka munthu asanayambe woneneredwayo kupenyana nao omnenera ndi kukhala napo podzikanira pa comneneraco.

17 Potero, pamene adasonkhana pano, sindinacedwa, koma m'mawa mwace ndinakhala pa mpando waciweruziro, ndipo ndinalamulira adze naye munthuyo.

18 Ndipo pamene anaimirira omneneza, sanamchulira konse cifukwa ca zoipa zonga ndinazilingirira ine;

19 koma anali nao mafunso ena otsutsana naye a cipembedzero ca iwo okha, ndi mafunso a wina Yesu, amene adafa, amene Paulo anati kuti ali ndi moyo.

20 Ndipo ine posinkhasinkha za mafunso awa ndinamfunsa ngati afuna kupita ku Yerusalemu, ndi kuweruzidwa komweko za izi.

21 Koma pakunena Paulo ndi kuti, asungidwe, akaturukire kwa Augusto, ndinaweruza asungidwe iye kufikira ndikamtumiza kwa Kaisara.

22 Ndipo Agripa anati kwa Festo, Ndifuna nanenso ndimve munthuyo. Anati, Mawa mudzamva iye.

23 M'mawa mwace tsono, atafika Agripa ndi Bemike ndi cifumu cacikuru, ndipo atalowa momvera milandu, pamodzi ndi akapitao akuru, ndi amuna omveka a mudziwo, ndipo pakulamulira Festo, anadza naye Paulo.

24 Ndipo Festo anati, Mfumu Agripa, ndi amuna inu nonse muli nafe pano pamodzi, muona uyu, amene unyinji wonse wa Ayuda anandiuza za iye, ku Yerusalemu ndi kunonso, ndi kupfuula kuti sayeneranso kukhala ndi moyo.

25 Koma ndinapeza ine kuti sanacita kanthu, koyenera imfa iye; ndipo popeza, iye yekha anati akaturukire kwa Augusto, ndatsimikiza mtima kumtumizako.

26 Koma ndiribe ine kanthu koti ndinenetse za iye kakulembera kwa mbuye wanga. Cifukwa cace ndamturutsira kwa inu, ndipo makamaka kwa inu, Mfumu Agripa, kuti, ndikatha kumfunsafunsa, ndikhale nako kanthu kakulembera.

27 Pakuti cindionekera copanda nzeru, potumiza wam'nsinga, wosachulanso zifukwa zoti amneneze.

26

1 Ndipo Agripa anati kwa Paulo, Kwaloleka udzinenere wekha. Pamenepo Paulo, anatambasula dzanja nadzikanira:

2 Ndidziyesera wamwai, Mfumu Agripa, popeza nditi ndidzikanira lero pamaso panu, za zonse zimene Ayuda andinenera nazo;

3 makamaka popeza mudziwitsa miyambo yonse ndi mafunso onse a mwa Ayuda; cifukwa cace ndikupemphani mundimvere ine moleza mtima.

4 Mayendedwe a moyo wanga tsono, kuyambira pa cibwana canga, amene anakhala ciyambire mwa mtundu wanga m'Yerusalemu, awadziwa Ayuda onse;

5 andidziwa ine ciyambire, ngati afuna kucitapo umboni, kuti ndinakhala Mfarisi monga mwa mpatuko wolunjikitsitsa wa cipembedzero cathu.

6 Ndipo tsopano ndiimirira pano ndiweruzidwe pa ciyembekezo ca lonjezano limene Mulungu analicita kwa makolo athu;

7 kunkira komweko mafuko athu khumi ndi awiri, potumikira Mulungu kosapumula usiku ndi usana, ayembekeza kufikirako. Cifukwa ca ciyembekezo ici, Mfumu, andinenera Ayuda.

8 Muciyesa cinthu cosakhulupirika, cakuti Mulungu aukitsa akufa?

9 Inedi ndinayesa ndekha, kuti kundiyenera kucita zinthu zambiri zotsutsana nalo dzina la Yesu Mnazarayo.

10 Cimenenso ndinacita m'Yerusalemu: ndipo ndinatsekera ine oyera mtima ambiri m'ndende, popeza ndidalandira ulamuliro wa kwa ansembe akulu; ndiponso pophedwa iwo, ndinabvomerezapo.

11 Ndipo ndinawalanga kawiri kawiri m'masunagoge onse, ndi kuwakakamiza anene zamwano; ndipo pakupsa mtima kwakukuru pa iwo ndinawalondalonda ndi kuwatsata ngakhale kufikira ku midzi yakunja.

12 M'menemo popita ine ku Damasiko ndi ulamuliro ndi ukumu wa kwa ansembe akulu, dzuwa lamsana,

13 ndinaona panjira, Mfumu, kuunika kocokera kumwamba kowalitsa koposa dzuwa, kunawala pondizinga ine ndi iwo akundiperekeza.

14 Ndipo pamene tidagwa pansi tonse, ndinamva mau akunena kwa ine m'cinenedwe ca Cihebri, Saulo, Saulo, undilondalonderanji Ine? nkukubvuta kutsalima pacothwikira.

15 Ndipo ndinati, Ndinu yani Mbuye? Ndipo Ambuye anati, Ine ndine Yesu amene iwe umlondalonda.

16 Komatu uka, imirira pa mapazi ako; pakuti cifukwa ca ici ndinaonekera kwa iwe, kukuika iwe ukhale mtumiki ndi mboni ya izi wandionamo Ine, ndiponso ya izi ndidzakuonekeramo we;

17 ndi kukulanditsa kwa anthu, ndi kwa amitundu, amene Ine ndikutuma kwa iwo,

18 kukawatsegulira maso ao, kuti atembenuke kucokera kumdima, kulinga kukuunika, ndi kucokera ulamuliro wa Satana kulinga kwa Mulungu, kuti alandire iwo cikhululukiro ca macimo, ndi colowa mwa iwo akuyeretsedwa ndi cikhulupiriro ca mwa Ine.

19 Potero, Mfumu Agripa, sindinakhala ine wosamvera masomphenya a Kumwamba;

20 komatu kuyambira kwa iwo a m'Damasiko, ndi a m'Yerusalemu, ndi m'dziko lonse la Yudeya, ndi kwa amitundunso ndinalalikira kuti alape, natembenukire kwa Mulungu, ndi kucita nchito zoyenera kutembenuka mtima.

21 Cifukwa ca izi Ayuda anandigwira m'Kacisi, nayesa kundipha.

22 Pamenepo pothandizidwa ndi Mulungu, ndiimirira kufikira lero lino, ndi kuwacitira umboni ang'ono ndi akuru, posanena kanthu kena koma zimene aneneri ndi Mose ananenazidzafika;

23 kuti Kristu akamve zowawa, kuti iye, woyamba mwa kuuka kwa akufa, adzalalikira kuunika kwa anthu ndi kwa amitundu.

24 Koma pakudzikanira momwemo, Festo anati ndi mau akuru, Uli wamisala Paulo; kuwerengetsa kwako kwakucititsa misala.

25 Koma Paulo anati, Ndiribe misala, Festo womvekatu; koma nditurutsa mau a coonadi ndi odziletsa.

26 Pakuti mfumuyo idziwa izi, kwa iye imene ndilankhula nayonso mosaopa: pakuti ndidziwadi kuti kulibe kanthu ka izi kadambisikira; pakuti ici Sicinacitika m'tseri.

27 Mfumu Agripa, mukhulupirira aneneri kodi? ndidziwa kuti muwakhulupirira.

28 Ndipo Agripa anati kwa Paulo, Ndi kundikopa pang'ono ufuna kundiyesera Mkristu.

29 Ndipo Paulo anati, Mwenzi atalola Mulungu, kuti ndi kukopa pang'ono, kapena ndi kukopa kwambiri, si inu nokha, komatunso onse akundimva ine lero, akadakhala otero onga ndiri ine, osanena nsinga izi.

30 Ndipo ananyamuka mfumu, ndi kazembe, ndi Bemike, ndi iwo akukhala nao;

31 ndipo atapita padera analankhula wina ndi mnzace, nanena, Munthu uyu sanacita kanthu koyenera imfa, kapena nsinga.

32 Ndipo Agripa anati kwa Festo, Tikadakhoza kumasula munthuyu, wakadapanda kunena, Ndikaturukire kwa Kaisara.

27

1 Ndipo pamene padatsimikizika kuti tipite m'ngalawa kunka ku Italiya, anapereka Paulo ndi andende ena kwa kenturiyo dzina lace Yuliyo, wa gulu la Augusto.

2 Ndipo m'mene tidalowam'ngalawa ya ku Adramutiyo ikati ipite kunka ku malo a ku mbali ya Asiya, dnakankha, ndipo Aristarko Mmakedoniya wa ku Tesalonika, anali nafe.

3 Ndipo m'mawa mwace tinangokoceza ku Sidoni; ndipo Yuliyo anacitira Paulo mwacikondi, namlola apite kwa abwenzi ace amcereze.

4 Ndipo pokankhanso pamenepo, tinapita kutseri kwa Kupro, popeza mphepo inaomba mokomana nafe.

5 Ndipo pamene tidapyola nyanja ya kunsi kwace kwa Kilikiya ndi Pamfiliya, tinafika ku Mura wa Lukiya.

6 Ndipo kenturiyo anapezako ngalawa ya ku Alesandriya, irikupita ku Italiya, ndipo anatilongamo.

7 Ndipo m'mene tidapita pang'ono pang'ono masiku ambiri, ndi kufika mobvutika pandunji pa Knido, ndipo popeza siinatilolanso mphepo, tinai pita m'tseri mwa Krete, pandunji pa Salimone;

8 ndipo popaza-pazapo mobvutika, tinafika ku malo ena dzina lace Pokoceza Pokoma; pafupi pamenepo panali mudzi wa Laseya.

9 Ndipo Itapita nthawi yambiri, ndipo unayambokhala woopsya ulendowo, popezanso nyengo ya kusala cakudya idapita kale, Paulo anawacenjeza,

10 nanena nao, Amuna inu, ndiona ine kuti ulendo udzatitengera kuonongeka ndi kutayika kwambiri, si kwa akatundu okha kapena ngalawa yokha, komatunso kwa moyo wathu.

11 Koma kenturiyo anakhulupirira watsigiro ndi mwini ngalawa makamaka, wosasamala mau a Paulo.

12 Ndipo popezadooko silinakoma kugonapo nyengo yacisanu, unyinji unacita uphungu ndi kutiamasule nacokepo, ngati kapena nkutheka afikire ku Foinika, ndi kugonako, ndilo dooko la ku Krete, loloza kumpoto ndi kumwela.

13 Ndipo poomba pang'ono mwela, poyesa kuti anaona cofunirako, anakoka nangula, napita m'mbali mwa Krete.

14 Koma patapita pang'ono idaombetsa kucokerako mphepo ya namondwe, yonenedwa Eurokulo;

15 ndipo pogwidwa nayo ngalawa, yosakhoza kupitanso mokomana nayo mphepo, tidangoleka, ndipo tinangotengedwa.

16 Ndipo popita kutseri kwa cisumbu cacing'ono dzina lace Kauda, tinakhoza kumangitsa bwato koma mobvutika;

17 ndipo m'mene adaukweza, anacita nazo zothandizira, nakulunga ngalawa; ndipo pakuopa kuti angatayike pa Surti, anatsitsa matanga, natengedwa motero.

18 Ndipo pobvutika kwakukuru ndi namondweyo, m'mawa mwace anayamba kutaya akatundu;

19 ndipo tsiku lacitatu anataya ndi manja ao a iwo eni zipangizo za ngalawa.

20 Ndipo m'mene dzuwa kapena nyenyezi sizinatiwalira masiku ambiri, ndipo namondwe wosati wamng'ono anatigwera, ciyembekezo conse cakuti tipulumuke cidaticokera pomwepo.

21 Ndipo pamene atakhala nthawi yaikuru osadya kanthu, Paulo anaimirira pakati pao, nati, Amuna inu, mukadamvera ine, osacoka ku Krete, osadzitengera kuonongeka ndi kutayika kumene.

22 Koma tsopano ndikucenjezani mulimbike mtima; pakuti sadzatayika wamoyo mmodzi mwa inu, koma ngalawa ndiyo.

23 Pakuti anaimirira kwa ine usiku walero mngelo wa Mulungu amene ndiri wace, amenenso ndimtumikira,

24 nanena, Usaope Paulo; ukaimirira pamaso pa Kaisara; ndipo, taona, Mulungu anakupatsa onse amene akuyenda nawe pamodzi.

25 Cifukwa cace, limbikani mtima, amuna inu; pakuti ndikhulupirira Mulungu, kuti kudzatero monga momwe ananena ndi ine.

26 Koma tiyenera kutayika pa cisumbu cakuti.

27 Koma pofika usiku wakhumi ndi cinai, potengedwa ife kwina ndi kwina m'nyanja ya Adriya, pakati pa usiku amarinyero anazindikira kuti analikuyandikira kumtunda;

28 ndipo anayesa madzi, napeza mikwamba makumi awiri; ndipo katapita kanthawi, anayesanso, napeza mikwamba khumi ndi isanu.

29 Ndipo pakuopa tingatayike pamiyala, anaponya anangula anai kumakaliro, nakhumba kuti kuce.

30 Ndipo m'mene amarinyero anafunakuthawa m'ngalawa, natsitsira bwato m'nyanja, monga ngati anati aponye anangula kulikuru,

31 Paulo anati kwa kenturiyo ndi kwa asilikari, Ngati awa sakhala m'ngalawa inu simukhoza kupulumuka.

32 Pamenepo asilikari anadula zingwe za bwato, naligwetsa.

33 Ndipo popeza kulinkuca, Paulo anawacenjeza onse adye kanthu, nati, Lero ndilo tsiku lakhumi ndi cinai limene munalindira, ndi kusala cakudya, osalawa kanthu.

34 Momwemo ndikucenjezani mutenge kanthu kakudya; pakuti kumeneku ndi kwa cipulumutsocanu; pakuti silidzatayika tsitsi la pa mutu wa mmodzi wa inu.

35 Ndipo atanena izi, ndi kutenga mkate, anayamika Mulungu pamaso pa onse; ndipo m'mene adaunyema anayamba kudya.

36 Ndipo anakhala olimbika mtima onse, natenga cakudya iwo omwe.

37 Ndipo life tonse tiri m'ngalawa ndife anthu mazana awiri mphambu makumi asanu ndi awiri kudza asanu ndi mmodzi.

38 Ndipo m'mene anakhuta, anapepuza ngalawa, nataya tirigu m'nyarija.

39 Ndipo kutaca sanazindikira dzikolo; koma anaona pali bondo la mcenga; kumeneko anafuna, ngati nkutheka, kuyendetsako ngalawa.

40 Ndipo m'mene anataya anangula anawasiya m'nyanja, namasulanso zingwe zomanga tsigiro; ndipo pokweza thanga la kulikuru, analunjikitsa kumcenga.

41 Koma pofika pamalo pokomana mafunde awiri, anatsamitsapo ngalawa; ndipo kulikuru kunatsama, ndi kukhala kosasunthika, koma kumakaliro kunasweka ndi mphamvu ya mafunde.

42 Ndipo uphungu wa asilikari udati awapheandende, angasambire, ndi kuthawa.

43 Koma kenturiyo, pofuna kupulumutsa Paulo, anawaletsa angacite ca uphungu wao; nalamula kuti iwo akukhoza kusambira ayambe kudziporiya m'nyanja, nafike pamtunda,

44 ndipo otsalawo, ena pamatabwa, ndi ena pa zina za m'ngalawa. Ndipo kudatero kuti lonse adapulumukira pamtunda.

28

1 Ndipo titapulumuka, pamenepo tinadziwa kuti cisumbuco cinachedwa Melita.

2 Ndipo akunja anaticitira zokoma zosacitika pena ponsepo; pakuti anasonkha moto, natilandira ife tonse, cifukwa ca mvula inalinkugwa, ndi cifukwa ca cisanu.

3 Koma pamene Paulo adaola cisakata ca nkhuni, naciika pamoto, inaturukamo njoka, cifukwa ca kutenthaku, nilumadzanja lace.

4 Koma pamene akunjawo anaona ciromboco ciri lende pa dzanja lace, ananena wina ndi mnzace, Zoona munthuyu ndiye wambanda, angakhale anapulumuka m'nyanja, cilungamo sicimlola akhale ndi moyo.

5 Koma anakutumulira ciromboco kumoto, osamva kupweteka.

6 Koma anayesa kuti adzatupa, kapena mwini wace kugwa kufa pomwepo; koma m'mene adalindira nthawitu, naona kuti sikunampweteka, anapindula, nati, Ndiye Mulungu.

7 Koma pafupt pamenepo panali minda, mwini wace ndiye mkulu cisumbuco, dzina lace Popliyo; amene anatilandira ife, naticereza okoma masiku atatu.

8 Ndipo kunatero kuti atate wace wa Popliyo anagona wodwala nthenda ya malungo ndi kamwazi. Kwa iyeyu Paulo analowa, napemphera, naika manja pa iye, namciritsa.

9 Ndipo patacitika ici, enanso a m'cisumbu, okhala nazo nthenda, anadza, naciritsidwa;

10 amenenso anaticitira ulemu wambiri; ndipo pocoka ife anatiikira zotisowa.

11 Ndipo itapita miyezi itatu tinayenda m'ngalawa ya ku Alesandriya, idagonera nyengo ya cisanu kucisumbuko, cizindikilo cace, Ana-a-mapasa.

12 Ndipo pamene tinakoceza ku Surakusa, tinatsotsako masiku atatu.

13 Ndipo pocokapo tinapaza ntifika ku Regio; ndipo litapita tsiku limodzi unayamba mwela, ndipo m'mawa mwace tinafika ku Potiyolo:

14 pamenepo tinakomana ndi abale, amene anatiumirira tikhale nao masiku asanu ndi awiri; ndipo potero tinafika ku Roma.

15 Kucokera kumeneko abalewo, pakumva za ife, anadza kukomana nafe ku Bwalo la Apiyo, ndi ku Nyumba za Alendo Zitatu; ndipo pamene Paulo anawaona, anayamika Mulungu, nalimbika mtima.

16 Ndipo pamene tinalowa m'Roma, analola Paulo akhale pa yekha ndi msilikari womdikira iye.

17 Ndipo kunali, atapita masiku atatu, anaitana akulu a Ayuda asonkhane; ndipo atasonkhana, ananena nao, Ine, amuna, abale, ndingakhale sindinacita kanthu kakuipsa anthu, kapena miyambo ya makolo, anandipereka wam'nsinga kucokera ku Yerusalemu ku manja a Aroma;

18 ndiwo, atandifunsafunsa ine anafuna kundimasula, popeza panalibe cifukwa ca kundiphera.

19 Koma pakukanapo Ayuda, ndinafulumidwa mtima kuturukira kwa Kaisara; si kunena kuti ndinali nako kanthu kakunenera mtundu wanga.

20 Cifukwa ca ici tsono ndinakupemphani inu mundione ndi kulankhula nane; pakuti cifukwa ca ciyembekezo ca Israyeli ndamangidwa ndi unyolo uwu.

21 Ndipo anati kwa iye, Ife sitinalandira akalata onena za inu ocokera ku Yudeya, kapena sanadza kuno wina wa abale ndi kutiuza kapena kulankhula kanthu koipa ka inu.

22 Koma tifuna kumva mutiuze muganiza ciani; pakuti za mpatuko uwu, tidziwa kuti aunenera ponse ponse.

23 Ndipo pamene adampangira tsiku, anadza ku nyumba yace anthu ambiri; amenewo anawafotokozera, ndikucitira umboni Ufumu wa Mulungu, ndi kuwakopa za Yesu, zocokera m'cilamulo ca Mose ndi mwa aneneri, kuyambira mamawa kufikira madzulo.

24 Ndipo ena anamvera zonenedwazo, koma ena sanamvera.

25 Koma popeza sanabvomerezana, anacoka atanena Paulo mau amodzi, kuti, Mzimu Woyera analankhula kokoma mwa Yesaya Mneneri kwa makolo anu,

26 ndi kuti, Pita kwa anthu awa, nuti, Ndi kumva mudzamva, ndipo simudzazindikira konse; Ndipo pakupenya mudzapenya, koma osaona konse;

27 Pakuti mtima wa anthu awa watupatu, Ndipo m'makutu mwao mmolemakumva, Ndipo masoao anawatseka; Kuti angaone ndi maso, Nangamve ndi makutu, Nangazindikire ndi mtima, Nangatembenuke, Ndipo Ine ndingawaciritse.

28 Potero, dziwani inu, kuti cipulumutso ici ca Mulungu citumidwa kwa amitundu; iwonsoadzamva. [

29 ]

30 Ndipo anakhala zaka ziwiri zamphumphu m'nyumba yace yobwereka, nalandira onse akufika kwa iye,

31 ndi kulalikira Ufumu wa Mulungu, ndi kuphunzitsa za Ambuye Yesu Kristu ndi kulimbika konse, wosamletsa munthu.