1 MAU a Yehova amene anadza kwa Hoseya mwana wa Beeri masiku a Uziya, Yotamu, Ahazi, ndi Hezekiya, mafumu a Yuda, ndi masiku a Yerobiamu mwana wa Yoasi mfumu ya Israyeli.
2 Ciyambi ca kunena kwa Yehova mwa Hoseya, Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, Muka, udzitengere mkazi wacigololo ndi ana acigololo; pakuti dziko latsata cigololo cokha cokha kuleka kutsata Yehova.
3 Ndipo anamuka natenga Gomeri mwana wamkazi wa Diblaimu; iye naima, nambalira mwana wamwamuna.
4 Ndipo Yehova anati kwa iye, Umuche dzina lace Yezreeli; pakuti katsala kanthawi, ndipo ndidzabwezera cilango mwazi wa Yezreeli pa nyumba ya Yehu, ndi kuleketsa ufumu wa nyumba ya Israyeli.
5 Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo, ndidzatyola uta wa Israyeli m'cigwa ca Yezreeli.
6 Ndipo anaimanso, nabala mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa iye, Umuche dzina lace Wosacitidwacifundo; pakuti sindidzacitiranso cifundo nyumba ya Israyeli, kuti ndiwakhululukire konse.
7 Koma ndidzacitira cifundo nyumba ya Yuda, ndi kuwapulumutsa mwa Ine Yehova Mulungu wao, osawapulumutsa ndi uta, kapena lupanga, kapena nkhondo ndi akavalo, kapena apakavalo.
8 Ataleka tsono kuyamwitsa Wosacitidwa cifundo, anaima, nabala mwana wamwamuna.
9 Ndipo Yehova anati, Umuche dzina lace Si-anthuanga; pakuti inu sindinu anthu anga, ndipo Ine sindine wanu.
10 Angakhale anatero, kuwerenga kwace kwa ana a Israyeli kudzanga mcenga wa kunyanja, wosayeseka kapena kuwerengeka; ndipo kudzatero kuti m'mene adawanena, Simuli anthu anga, adzanena nao, Muli ana a Mulungu wamoyo.
11 Ndipo ana a Yuda ndi ana a Israyeli adzasonkhanidwa pamodzi, nadzadziikira mkuru mmodzi, nadzakwera kucoka m'dziko; pakuti tsiku la Yezreeli ndi lalikuru.
1 Nenani kwa abale anu, Anthu anga, ndi kwa alongo anu, Wocitidwa-cifundo.
2 Mutsutsane naye mai wanu, mutsutsane naye; pakuti sali mkazi wanga, ndi Ine sindiri mwamuna wace; ndipo acotse zadama zace pankhope pace, ndi zigololo zace pakati pa maere ace;
3 ndingambvule wamarisece, ndi kumuika ngati tsiku lija anabadwalo, ndi kumsanduliza ngati cipululu, ndi kumuika ngati dziko louma, ndi kumupha nalo ludzu;
4 ndipo ana ace sindidzawacitira cifundo; pakuti iwo ndiwo ana acigololo.
5 Pakuti mai wao anacita cigololo; iye amene anali ndi pakati pa iwo anacita camanyazi; pakuti anati, Ndidzatsata ondikondawo, akundipatsa ine cakudya canga, ndi madzi anga, ubweya wanga, ndi thonje langa, mafuta anga, ndi cakumwa canga.
6 Cifukwa cace taonani, ndidzacinga njira yako ndi minga, ndipo ndidzammangira mpanda, kuti asapeze mabande ace.
7 Ndipo adzatsata omkonda koma osawakumika, adzawafunafuna koma osawapeza; pamenepo adzati, Ndidzamuka ndi kubwererana ndi mwamuna wanga woyamba, popeza pamenepo panandikomera koposa tsopano.
8 Pakuti sanadziwa kuti ndine ndinampatsa tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta, ndi kumcurukitsira siliva ndi golidi, zimene anapanga nazo Baala.
9 Cifukwa cace ndidzabwera ndi kucotsa tirigu wanga m'nyengo yace, ndi vinyo wanga m'nthawi yace yoikika, ndi kukwatula ubweya wanga ndi thonje langi, zimene zikadapfunda umarisece wace.
10 Ndipo tsopano ndidzaonetsa manyazi ace pamaso pa omkonda, popandanso wakumlanditsa m'dzanja langa.
11 Ndidzaleketsanso kusekerera kwace konse, madyerero ace, pokhala mwezi pace, ndi masabata ace, ndi masonkhano ace onse oikika.
12 Ndipo ndidzapasula mipesa yace ndi mikuyu yace, imene adanena, Iyi ndi mphotho yanga anandipatsa ondikondawo; ndipo ndidzaisandutsa thengo, ndi nyama zakuthengo zidzaidya.
13 Ndipo ndidzamlanga cifukwa ca masiku a Abaala amene anawafukizira, nabvala mphete za m'mphuno, ndi zokometsera zace, natsata omkonda, nandiiwala Ine, ati Yehova.
14 Cifukwa cace taonani, ndidzamkopa ndi kumka naye kucipululu, ndi kulankhula naye momkonda mtima.
15 Ndipo ndidzampatsa minda yace yamphesa kuyambira pomwepo, ndi cigwa ca Akori cikhale khomo la ciyembekezo; ndipo adzabvomereza pomwepo monga masiku a ubwana wace, ndi monga tsiku lokwera iye kuturuka m'dziko la Aigupto.
16 Ndipo kudzakhala tsiku lomwelo, ati Yehova, udzandicha Mwamuna wanga, osandichanso Baala wanga.
17 Pakuti ndidzacotsa maina a Abaala m'kamwa mwace; ndipo silidzakumbukikanso dzina lao.
18 Ndipo tsiku lomwelo ndidzawacitira pangano ndi nyama za kuthengo, ndi mbalame za mlengalenga, ndi zokwawa pansi; ndipo ndidzatyola uta, ndi lupanga, ndi nkhondo, zicoke m'dziko, ndi kuwagonetsa pansi mosatekeseka.
19 Ndipo ndidzakutomera ukhale wanga kosatha, inde ndidzakutomera ukhale wanga m'cilungamo, ndi m'ciweruzo, ndi m'ukoma mtima, ndi m'cifundo.
20 Ndidzakutomeranso ukhale wanga mokhulupirika, ndipo udzadziwa Yehova.
21 Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo, ndidzabvomereza, ati Yehova, ndidzabvomereza thambo, ndi ilo lidzabvomereza dziko lapansi;
22 ndi dziko lapansi lidzabvomereza tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta; ndi izi zidzabvomereza Yezreeli.
23 Ndipo ndidzadzibzalira iye m'nthaka, ndipo ndidzacitira cifundo Wosacitidwa-cifundo; ndipo ndidzati kwa Si-anthu-anga, Muli anthu anga; ndipo iwo adzati, Ndinu Mulungu wathu.
1 Ndipo Yehova anati kwa ine, Mukanso, konda mkazi wokondedwa ndi bwenzi lace, koma wakucita cigololo monga Yehova akonda ana a Israyeli, angakhale atembenukira ku milungu yina, nakonda ncinci za mphesa zouma.
2 M'mwemo ndinadzigulira iye ndi ndalama khumi ndi zisanu zasiliva, ndi homeri ndi nusu wa barele;
3 ndipo ndinati kwa iye, Uzikhala ndi ine masiku ambiri, usacita cigololo, usakhala mkazi wa mwamuna ali yense; momwemo inenso nawe.
4 Pakuti ana Israyeli adzakhala masiku ambiri a opanda mfumu, ndi opanda kalonga, ndi opanda nsembe, ndi opanda coimiritsa, ndi opanda efodi kapena aterafi;
5 atatero ana a Israyeli adzabwera, nadzafuna Yehova Mulungu wao, ndi Davide mfumu yao, nadzafika ndi mantha kwa Yehova, ndi ku ukoma wace masiku otsiriza.
1 Imvani mau a Yehova, inu ana a Israyeli; pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi okhala m'dziko, popeza palibe coonadi, kapena cifundo, kapena kudziwa Mulungu m'dziko.
2 Koma kulumbira, ndi kunama, ndi kupha, ndi kuba, ndi kucita cigololo; aboola, ndi mwazi ukhudzana nao mwazi.
3 Cifukwa cace dziko lidzacita cisoni, ndi ali yense wokhalamo adzalefuka, pamodzi ndi nyama za kuthengo, ndi mbalame za m'mlengalenga; ndi nsomba za m'nyanja zomwe zidzacotsedwa.
4 Koma munthu asatsutsane ndi mnzace, kapena kudzudzula mnzace; popeza anthu ako ndiwo akunga otsutsana ndi wansembe.
5 Ndipo udzakhumudwa usana, ndi mneneri yemwe adzakhumudwa pamodzi ndi iwe usiku; ndipo ndidzaononga mai wako.
6 Anthu anga aonongeka cifukwa ca kusadziwa; popeza unakana kudziwa, Inenso ndikukaniza, kuti usakhale wansembe wanga; popeza waiwala cilamulo ca Mulungu wako, Inenso ndidzaiwala ana ako.
7 Monga anacuruka, momwemo anandicimwira; ndidzasanduliza ulemerero wao ukhale manyazi.
8 Adyerera cimo la anthu anga, nakhumbira cosalungama cao, yense ndi mtima wace.
9 Ndipo kudzakhala monga anthu, momwemo wansembe; ndipo ndidzawalanga cifukwa canjira zao, ndi kuwabwezera macitidwe ao.
10 Ndipo adzadya, koma osakhuta; adzacita cigololo, koma osacuruka; pakuti waleka kusamalira Yehova.
11 Cigololo, ndi vinyo, ndi vinyo watsopano, zicotsa mtima,
12 Anthu anga afunsira ku mtengo wao, ndi ndodo yao iwafotokozera; pakuti mzimu wacigololo wawalakwitsa, ndipo acita cigololo kucokera Mulungu wao.
13 Pamwamba pa mapiri aphera nsembe, nafukiza pazitunda, patsinde pa thundu, ndi miniali, ndi mkundi; popeza mthunzi wace ndi wabwino, cifukwa cace ana anu akazi acita citole, ndi apongozi anu acita cigololo.
14 Sindidzalanga ana anu akazi pocita citole iwo, kapena apongozi anu pocita cigololo iwo; pakuti iwo okha apambukira padera ndi akazi acitole, naphera nsembe pamodzi ndi akazi operekedwa kucitole; ndi anthu osazindikirawo adzagwetsedwa camutu.
15 Cinkana iwe, Israyeli, ucita citole, koma asaparamule Yuda; ndipo musafika inu ku Giligala, kapena kukwera ku Betaveni, kapena kulumbira, Pali Yehova.
16 Pakuti Israyeli wacita kuuma khosi ngati ng'ombe yaikazi yaing'ono youma khosi; tsopano Yehova adzawadyetsa ngati mwana wa nkhosa ku thengo lalikuru.
17 Efraimu waphatikana ndi mafano, mlekeni.
18 Cakumwa cao casasa, acita citole kosalekeza; akuru ao akonda manyazi kwambiri.
19 Mphepo yamkulunga m'mapiko ace, ndipo adzacita manyazi cifukwa ca nsembe zao.
1 Imvani ici, ansembe inu; mverani, inu nyumba ya Israyeli; cherani khutu, inu nyumba ya mfumu; pakuti ciweruzoci cinena inu; pakuti munakhala msampha ku Mizipa, ndi ukonde woyalidwa pa Tabora.
2 Ndipo opandukawo analowadi m'zobvunda; koma Ine ndine wakuwadzudzula onsewo.
3 Ndimdziwa Efraimu, ndi Israyeli sandibisikira; pakuti Efraimu iwe, wacita citole tsopano, Israyeli wadetsedwa.
4 Macitidwe ao sawalola kubwerera kwa Mulungu wao; pakuti mzimu wacitole uli m'kati mwao, ndipo sadziwa Yehova.
5 Ndipo kudzikuza kwa Israyeli kudzamcitira umboni pamaso pace; cifukwa cace Israyeli ndi Efraimu adzakhumudwa m'mphulupulu mwao; Yudanso adzakhumudwa pamodzi nao.
6 Adzamuka ndi zoweta zao zazing'ono ndi zazikuru kufunafuna Yehova: koma sadzampeza; Iye wadzibweza kuwacokera.
7 Anacita mosakhulupirika pa Yehova, pakuti anabala ana acilendo; mwezi wokhala udzawatha tsopano, pamodzi ndi maiko ao.
8 Ombani mphalasa m'Gibeya, ndi lipenga m'Rama; pfuulani ku Betaveni; pambuyo pako, Benjamini.
9 Efraimu adzasanduka bwinja tsiku lakudzudzula; mwa mapfuko a Israyeli ndadziwitsa codzacitikadi.
10 Akalonga a Yuda akunga anthu osuntha malire; ndidzawatsanulira mkwiyo wanga ngati madzi.
11 Efraimu azunzika, apsinjika pa mlanduwo; pakuti anafuna mwini wace kutsata lamulolo.
12 Ndipo ndikhala kwa Efraimu ngati njenjete, ndi kwa nyumba ya Yuda ngati cibvundi.
13 Pamene Efraimu anaona nthenda yace, ndi Yuda bala lace, Efraimu anamuka kwa Asuri, natumiza kwa mfumu Yarebu; koma iye sakhoza kukuciritsani, kapena kupoletsa bala lanu.
14 Pakuti ndidzakhala kwa Efraimu ngati mkango, ndi kwa nyumba ya Yuda ngati msona wa mkango; ndidzamwetula Ine ndi kucoka; ndidzanyamula, ndipo palibe wakulanditsa.
15 Ndidzamuka ndi kubwerera kumka kumalo kwanga, mpaka adzabvomereza kuparamula kwao, nafunafuna nkhope yanga; m'msauko mwao adzandifunafuna mwacangu.
1 Tiyeni, tibwerere kunka kwa Yehova; pakuti wang'amba, nadzatipoletsera; wakantha, nadzatimanga.
2 Atapita masiku awiri adzatitsitsimutsa, tsiku lacitatu adzatiutsa; ndipo tidzakhala ndi moyo pamaso pace.
3 Tidziwe tsono, tilondole kudziwa Yehova; kuturuka kwace kwakonzekeratu ngati matanda kuca; ndipo adzatidzera ngati mvula, ngati mvula ya masika yakuthirira dziko.
4 Efraimu iwe, ndidzakucitira ciani? Yuda iwe, ndikucitire ciani? pakuti kukoma mtima kwako kukunga mtambo wam'mawa ndi ngati mame akuphawa mamawa.
5 Cifukwa cace ndawalikha mwa aneneri; ndawapha ndi mau a pakamwa panga; ndi maweruzo anga aturuka ngati kuunika.
6 Pakuti ndikondwera naco cifundo, si nsembe ai; ndi kumdziwa Mulungu koposa nsembe zopsereza.
7 Koma iwo analakwira cipangano ngati Adamu, m'mene anandicitira monyenga.
8 Gileadi ndiwo mudzi wa ocita zoipa, wa mapazi a mwazi.
9 Ndipo monga magulu a mbala alalira munthu, momwemo msonkhano wa ansembe amapha pa njira ya ku Sekemu; indedi acita coipitsitsa.
10 M'nyumba ya Israyeli ndinaona cinthu coopsetsa; pamenepo pali citole ca Efraimu; Israyeli wadetsedwa.
11 Akuikidwiratunso nyengo yakukolola, Yuda iwe, pamene ndikabwezanso undende wa anthu anga.
1 M'mene ndiciritsa Israyeli, mphulupulu ya Efraimu ibvumbuluka, ndi zoipa za Samariya; pakuti acita bodza, ndipo mkhungu alowa m'nyumba, ndi gulu la mbala manca kubwalo.
2 Ndipo sanena m'mtima mwao kuti Ine ndikumbukila zoipa zao zonse; tsopano macitidwe ao awazinga; ali pamaso panga,
3 Akondweretsa mfumu ndi zoipa zao, ndi akalonga ndi mabodza ao.
4 Acigololo onsewo; akunga ng'anjo anaitenthetsa wooca mkate; aleka kusonkha moto, poyambira kukanda mtanda kufikira watupa mtandawo.
5 Tsiku la mfumu yathu akalonga adzidwalitsa ndi kutentha kwa vinyo; iye anatambasula dzanja lace pamodzi ndi oseka.
6 Pakuti asendera nao mtima wao wakunga ng'anjo ya mkate, pokhala alikulalira; wooca mkate wao agona usiku wonse, m'mawa iyaka ngati moto wa malawi.
7 Onsewo atentha ngati ng'anjo, natha oweruza ao, agwa mafumu ao onse; palibe mmodzi mwa iwo wakuitana Ine.
8 Efraimu asokonezana nayo mitundu ya anthu; Efraimu ndiye kamtanda ka mkate kosatembenuzidwa.
9 Alendo anatha mphamvu yace osacidziwaiye; imvi zomwe zampakiza osacidziwa iye,
10 Ndipo kudzikuza kwa Israyeli kumcitira umboni pamaso pace; koma sanabwerera kumka kwa Yehova Mulungu wao, kapena kumfunafuna mwa ici conse.
11 Ndipo Efraimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru; aitanira kwa Aigupto, amuka kwa Asuri.
12 Pamene amuka ndidzawayalira ukonde wanga, ndidzawagwetsa ngati mbalame za m'mlengalenga, ndidzawalanga monga udamva msonkhano wao.
13 Tsoka kwa iwowa! pakuti anandizembera; cionongeko kwa iwowa! pakuti anandilakwira; ndikadawalanditsa Ine, koma anandinenera zabodza.
14 Ndipo sanapfuulira kwa Ine ndi mtima wao, koma alira pakama pao, asonkhanira tirigu ndi vinyo, apikisana ndi Ine.
15 Cinkana ndawalangiza ndi kulimbitsa manja ao, andilingiririra coipa,
16 Abwerera, koma si kwa Wam'mwambayo; akunga uta wosakhulupirika; akalonga ao adzagwa ndi lupanga mwa cipongwe ca lilime lao; ici ndico adzawasekera m'dziko la Aigupto.
1 Lipenga kukamwa kwako, Akudza ngati ciombankhanga, kulim bana ndi nyumba ya Yehova; cifukwa analakwira cipangano canga, napikisana naco cilamulo canga.
2 Adzapfuulira kwa Ine, Mulungu wanga, ife Aisrayeli tikudziwani.
3 Israyeli wacitaya cokoma, mdani adzamlondola.
4 Analonga mafumu, koma sikunacokera kwa Ine; anaika akalonga, koma sindinadziwa; anadzipangira mafano a siliva wao ndi golidi wao, kuti akalikhidwe.
5 Mwana wa ng'ombe wako wakutaya, Samariya iwe; mkwiyo wanga wayakira iwo; adzalephera kuyera mtima mpaka liti?
6 Pakuti ici comwe cafumira kwa Israyeli; mmisiri wampanga, koma sali Mulungu; inde mwana wa ng'ombe wa Samariya adzaphwanyika-phwanyika.
7 Pakuti abzala mphepo, nadzakolola kabvumvulu; alibe tirigu wosasenga; ngala siidzaturutsa ufa; cinkana iuturutsa, alendo adzaumeza.
8 Israyeli wamezedwa; tsopano ali mwa amitundu ngati cotengera coti munthu sakondwera naco.
9 Pakuti anakwera kumka ku Asuri, ngati mbidzi ya pa yokha mwini wace; Efraimu walembera omkonda ngati anchito.
10 Inde angakhale alembera mwa amitundu ndidzawasonkhanitsa tsopano; ndipo ayamba kucepa cifukwa ca katundu wa mfumu ya akalonga.
11 Popeza Efraimu anacurukitsa maguwa a nsembe akucimwako, maguwa a nsembe omwewo anamcimwitsa.
12 Ndinamlembera zinthu zambirimbirizo za cilamulo canga, koma zinayesedwa ngati cinthu cacilendo.
13 Kunena za nsembe za zopereka zanga, aphera nsembe yanyama, naidya; koma Yehova sazilandira; tsopano adzakumbukila mphulupulu yao, nadzalanga zocimwa zao; adzabwerera kumka ku Aigupto.
14 Pakuti Israyeli waiwala Mlengi wace, namanga akacisit ndipo Yuda wacurukitsa midzi yamalinga; koma ndidzatumizira midzi yace moto, nudzatha nyumba zace zazikuru.
1 Usakondwera, Israyeli, ndi kusekerera, ngati mitundu ya anthu; pakuti wacita cigololo kuleka Mulungu wako, wakonda mphotho ya cigololo pa dwale la tirigu liri lonse.
2 Dwale ndi coponderamo mphesa sizidzawadyetsa, vinyo watsopano adzamsowa.
3 Sadzakhala m'dziko la Yehova; koma Efraimu adza bwerera kumka ku Aigupto; ndipo adzadya cakudya codetsa m'Asuri.
4 Sadzatsanulira Yehova nsembe zavinyo; sizidzamkomera Iye nsembe zao; zidzakhala kwa iwo ngati mkate wa acisoni; onse akudyako adzadetsedwa; pakuti mkate wao udzakhala wa njala yao, uwu sudzalowa m'nyumbaya Yehova.
5 Mudzacitanji tsiku la masonkhano oikika, ndi tsiku la madyerero a Yehova?
6 Pakuti taonani, anacokera cionongeko, koma Aigupto adzawasonkhanitsa, Mofi adzawaika m'manda; khwisa adzalanda zofunika zao zasiliva; minga idzakhala m'mahema mwao.
7 Masiku a kulanga afika, masiku a kubwezera afika; Israyeli adzadziwa; mneneri ali wopusa, munthu wamzimu ali wamisala, cifukwa ca kucuruka mphulupulu yako, ndi popeza udani ndi waukuru.
8 Efraimu ndiye wozonda kwa Mulungu wanga; kunena za mneneri, msampha wa msodzi uli m'njira zace zonse, ndi udani m'nyumba ya Mulungu wace.
9 Anadzibvunditsa kwambiri, monga masiku a Gibeya; adzakumbukila mphulupulu yao, adzalanga zocimwa zao.
10 Ndinapeza Israyeli ngati mphesa m'cipululu, ndinaona makolo anu ngati cipatso coyamba ca mkuyu nyengo yace yoyamba; koma anadza kwa Baala Peori, nadzipatulira conyansaco, nasandulika onyansa, conga cija anacikonda.
11 Kunena za Efraimu, ulemerero wao udzauluka ndi kucoka ngati mbalame; sipadzakhala kubala, ndi kukhala ndi pakati, ndi kuima.
12 Angakhale alera ana ao, koma ndidzawasowetsa, wosatsala munthu; ndithunso tsoka iwowa, pamene ndiwacokera.
13 Efraimu, monga ndaona, akunga Turo, wookedwa pokoma; koma Efraimu adzaturutsira ana ace wakuwaphera.
14 Apatseni, Yehova; mudzapatsa ciani? muwapatse mimba yotayataya, ndi mawere ouma.
15 Coipa cao conse ciri m'Giligala; pakutipamenepo ndinawada, cifukwa ca kuipa kwa macitidwe ao ndidzawainga kuwacotsa m'nyumba mwanga; sindidzawakondanso; akalonga ao onse ndiwo opanduka.
16 Efraimu wakanthidwa, muzu wao wauma, iwo sadzabala zipatso; inde ngakhale abala, koma ndidzapha zipatso zofunika za mimba yao.
17 Mulungu wanga adzawataya, pakuti sanammvera Iye; ndipo adzakhala othawathawa mwa amitundu.
1 Israyeli ndi mpesa wotambalala, wodzibalira wokha zipatso; monga umo zinacurukira zipatso zace, momwemo anacurukitsa maguwa a nsembe ace; monga mwa kukoma kwace kwa dziko lace anapanga zoimiritsa zokoma.
2 Mtima wao wagawikana, tsopano adzapezeka oparamula, adzapasula maguwa ao a nsembe, nadzaononga zoimiritsa zao.
3 Pakuti tsopano adzati, Tiribe mfumu, popeza sitiopa Yehova; ndi mfumu idzaticitira ciani?
4 Anena mau akulumbira monama, pakucita mapangano momwemo; ciweruzo ciphuka ngati zitsamba zowawa m'micera ya munda.
5 Okhala m'Samariya adzaopera cifanizo ca ana a ng'ombe a ku Betaveni; pakuti anthu ace adzamva naco cisoni, ndi ansembe ace amene anakondwera naco, cifukwa ca ulemerero wace, popeza unacicokera.
6 Adzacitengeranso ku Asuri cikhale mphatso ya kwa mfumu Yarebu; Efraimu adzatenga manyazi, ndi Israyeli adzacita manyazi ndi uphungu wace.
7 Ndipo Samariya, mfumu yace yamwelera ngati thobvu pamadzi.
8 Ndipo misanje ya Aveni, ndiyo cimo la Israyeli, idzaonongeka; minga ndi mitungwi idzamera pa maguwa ao a nsembe; ndipo adzati kwa mapiri, Tiphimbeni; ndi kwa zitunda, Tigwereni.
9 Israyeli, wacimwa kuyambira masiku a Gibeya; pomwepo anaimabe; nkhondo ya pa ana a cosalungama siinawapeza ku Gibeya.
10 Pamene ndifuna ndidzawalanga, ndi mitundu ya anthu idzawasonkhanira pomangidwa iwo pa zolakwa zao ziwiri.
11 Ndipo Efraimu ndiye ng'ombe yaikazi yaing'ono, yozereweredwa, yokonda kupuntha tirigu; koma ndapita pa khosi lace lokoma; ndidzamsenzetsa Efraimu goli; Yuda adzalima, Yakobo adzaphwanya cibuluma cace.
12 Mudzibzalire m'cilungamo mukolole monga mwa cifundo; limani masala anu, pakuti yafika nthawi ya kufuna Yehova, mpaka afika Iye, nabvumbitsira inu cilungamo.
13 Mwalima coipa, mwakolola cosalungama, mwadya zipatso za mabodza; pakati watama njira yako ndi kucuruka kwa anthu ako amphamvu.
14 Momwemo phokoso lidzaukira anthu ako, ndi malinga ako onse adzapasuka, monga Salimani anapasula Betaribeli; tsiku la nkhondo amai anaphwanyika pamodzi ndi ana ace.
15 Momwemo adzakucitirani Betele, cifukwa ca coipa canu cacikuru; mbanda kuca mfumu ya Israyeli idzalikhika konse.
1 Pamene Israyeli anali mwana, ndinamkonda, ndinaitana mwana wanga ali m'Aigupto.
2 Monga anawaitana, momwemo anawacokera; anaphera nsembe Abaala, nafukizira mafano osema.
3 Koma Ine ndinaphunzitsa Efraimu kuyenda, ndinawafungata m'manja mwanga; koma sanadziwa kuti ndinawaciritsa.
4 Ndinawakoka ndi zingwe za munthu, ndi zomangira za cikondi; ndinakhala nao ngati iwo akukweza goli pampuno pao, ndipo ndinawaikira cakudya.
5 Iye sadzabwerera kumka ku dziko la Aigupto, koma Asuri adzakhala mfumu yace, popeza anakana kubwera.
6 Ndi lupanga lidzagwera midzi yace, lidzatha mipiringidzo yace, ndi kuononga cifukwa ca uphungu wao.
7 Ndipo anthu anga alimbika kubwerera m'mbuyo kundileka Ine; cinkana akawaitana atsate Iye ali m'mwamba, sadzakweza ndi mmodzi yense.
8 Ndidzakusiya bwanji, Efraimu? ndidzakupereka bwanji, Israyeli? ndidzakuyesa bwanji ngati Adima? ndidzakuika bwanji ngati Zeboimu? mtima wanga watembenuka m'kati mwanga, zacifundo zanga zilira zonse pamodzi.
9 Sindidzacita mkwiyo wanga waukali, sindidzabwerera kuononga Efraimu; pakuti Ine ndine Mulungu, si munthu ai; Woyera wa pakati pako; ndipo sindidzalowa m'mudzi.
10 Adzatsata Yehova, Iye adzabangula ngati mkango; pamene abangula, ana adzafika ndi kunjenjemera kucokera kumadzulo.
11 Adzafika ndi kunjenjemera ngati mbalame ya ku Aigupto, ndi ngati nkhunda m'dziko la Asuri; ndipo ndidzawakhalitsa m'nyumba zao, ati Yehova.
12 Efraimu andizinga ndi bodza, ndi nyumba ya Israyeli ndi cinyengo, ndi Yuda apikisana ndi Mulungu, ndiye Woyera wokhulupirika.
1 Efraimu akudya mphepo, natsata mphepo ya kum'mawa; tsiku lonse acurukitsa mabodza ndi cipasuko, ndipo acita pangano ndi Asuri, natenga mafuta kumka nao ku Aigupto,
2 Ndipo Yehova ali ndi mlandu ndi Yuda, nadzalanga Yakobo monga mwa njira zace, adzambwezera monga mwa macitidwe ace.
3 M'mimba anagwira ku citende ca mkuru wace, ndipo atakula mphamvu analimbana ndi Mulungu;
4 inde, analimbana ndi wamthenga nampambana; analira, nampembedza Iye; anampeza Iye ku Beteli, ndi kumeneko Iye analankhula ndi ife;
5 ndiye Yehova Mulungu wa makamu, cikumbukilo cace ndi Yehova.
6 M'mwemo utembenukire kwa Mulungu wako, sunga cifundo ndi ciweruzo, nuyembekezere Mulungu wako kosalekeza.
7 Ndiye Mkanani, m'dzanja lace muli miyeso yonyenga, akonda kusautsa.
8 Ndipo Efraimu anati, Zedi ndasanduka wolemera, ndadzionera cuma m'nchito zonse ndinazigwira; sadzapeza mwa ine mphulupulu yokhala cimo.
9 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wako cicokere dziko la Aigupto, ndidzakukhalitsanso m'mahema, monga masiku a masonkhano oikika.
10 Ndalankhulanso ndi aneneri, ndipo Ine ndacurukitsa masomphenya; ndi pa dzanja la aneneri ndinanena ndi mafanizo.
11 Kodi Gileadi ndiye wopanda pace? akhala acabe konse; m'Giligala aphera nsembe yang'ombe; inde maguwa ao a nsembe akunga miulu yamiyala m'micera ya munda.
12 Ndipo Yakobo anathawira ku thengo la Aramu, ndi Israyeli anagwira nchito cifukwa ca mkazi, ndi cifukwa ca mkazi anaweta nkhosa.
13 Ndipo mwa mneneri Yehova anakweretsa Israyeli kucokera m'Aigupto, ndi mwa mneneri anasungika.
14 Efraimu wautsa mkwiyo wowawa, m'mwemo Iye adzamsiyira mwazi wace, ndi Ambuye wace adzambwezera comtonza cace.
1 Pamene Bfraimu analankhula panali kunjenjemera; anadzikweza m'Israyeli; koma pamene anaparamula mwa Baala, anafa.
2 Ndipo tsopano aonjeza kucimwa, nadzipangira mafano oyenga a siliva wao, mafano monga mwa nzeru zao, onsewo nchito ya amisiri; anena za iwo, Anthu ophera nsembe apsompsone ana a ng'ombe.
3 Cifukwa cace adzakhala ngati mtambo wa m'mawa, ndi ngati mame asansuka mamawa, ngati mungu umene mphepo iuuluza kudwale, ndi ngati utsi woturuka kukafwambira.
4 Koma Ine ndine Yehova Mulungu wako cicokere m'dziko la Aigupto, ndipo suyenera kudziwa mulungu wina koma Ine; ndi popanda Ine palibe mpulumutsi.
5 Ndinakudziwa m'cipululu, m'dziko lotentha kwambiri.
6 Monga mwa podyetsa pao, momwemo anakhuta; anakhuta, ndi mtima wao unakwezeka; cifukwa cace anandiiwala Ine.
7 Cifukwa cace ndikhala nao ngati mkango; ngati nyalugwe ndidzalalira kunjira.
8 Ndidzakomana nao ngati cimbalangondo cocilanda ana ace, ndi kung'amba cokuta mtima wao; ndi pomwepo ndidzawalusira ngati mkango; cirombo cidzawamwetula.
9 Israyeli, cikuononga ndi ici, cakuti utsutsana ndi Ine, cithandizo cako.
10 Iri kuti mfumu yako tsopano, kuti ikupulumutse m'midzi yako yonse? ndi oweruza ako amene unanena za iwo, Ndipatseni mfumu ndi akalonga?
11 Ndinakupatsa mfumu mu mkwiyo wanga; ndinamcotsanso m'ukali wanga.
12 Mphulupulu ya Efraimu yamangika, cimo lace lisungika.
13 Zowawa zonga za mkazi wobala zidzamgwera, ndiye mwana wopanda nzeru; pakuti pali nyengo yakuti asacedwe mobalira ana.
14 Ndidzawaombola ku, mphamvu ya kumanda, ndidzawaombola kuimfa; imfa, miliri yako iri kuti? manda, cionongeko cako ciri kuti? Kulekerera kudzabisika pamaso panga.
15 Cinkana abala mwa abale ace, mphepo ya kum'mawa idzafika, mphepo ya Yehova yokwera kucokera kucipululu; ndi gwero lace lidzaphwa, ndi kasupe wace adzauma, adzafunkha cuma ca akatundu onse ofunika.
16 Samariya adzasanduka wabwinja, pakuti anapandukana ndi Mulungu wace; iwo adzagwa ndi lupanga, ana ao amakanda adzaphwanyika, ndi akazi ao okhala ndi pakati adzatumbulidwa.
1 Israyeli, bwerera kumka kwa Yehova Mulungu wako; pakuti wagwa mwa mphulupulu yako.
2 Mukani nao mau, nimubwerere kwa Yehova; nenani kwa Iye, Cotsani mphulupulu zonse, nimulandire cokoma; ndipo tidzapereka mau milomo yathu ngati: ng'ombe.
3 Asuri sadzatipulumutsa; sitidzayenda pa akavalo, ndipo sitil dzanenanso kwa nchito ya manja athu, Inu ndinu milungu yathu; pakuti mwa Inu ana amasiye apeza cifundo.
4 Ndidzaciritsa kubwerera kwao, ndidzawakonda mwaufulu; pakuti mkwiyo wanga wamcokera.
5 Ndidzakhala kwa Israyeli ngati mame; adzacita maluwa ngati kakombo, ndi kutambalalitsa mizu yace ngati Lebano.
6 Nthambi zace zidzatambalala, ndi kukoma kwace kudzanga kwa mtengo waazitona, ndi pfungo lace ngati Lebano.
7 Iwo okhala pansi pa mthunzi wace adzabwera, nadzatsitsimuka ngati tirigu, nadzaphuka ngati mpesa, cikumbukilo cace cidzanga vinyo wa Lebano.
8 Efraimu adzati, Ndiri ndi cianinso ndi mafano? Ndayankha, ndidzampenyerera; ndiri ngati mtengo wamlombwa wabiriwiri; zipatso zako zipezeka zocokera kwa Ine.
9 Wanzeru ndani, kuti azindikire izi? waluntha, kuti adziwe izi? pakuti njira za Yehova ziri zoongoka; ndipo olungama adzayendamo, koma olakwa adzagwamo.