1

1 POPEZA ambiri anayesa kulongosola nkhani ya zinthu zinacitika pakati pa ife,

2 monga anazipereka kwa ife iwo amene anakhala mboni ndi atumiki a mau,

3 kuyambira paciyambi, ndinayesa nkokoma inenso, amene ndinalondalonda mosamalitsa zinthu zonse kuyambira paciyambi, kulembera kwa iwe tsatane tsatane, Teofilo wabwinotu iwe;

4 kuti udziwitse zoona zace za mau amene unaphunzira.

5 Masiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali munthu wansembe, dzina lace Zakariya, wa gulu la ansembe la Abiya; ndi mkazi wace wa ana akazi a pfuko la Aroni, dzina lace Elisabeti.

6 Ndipo onse awiri anali olungama mtima pamaso pa Mulungu, namayendabe m'malamulo onse ndi zoikika za Ambuye osacimwa.

7 Ndipo analibe mwana, popeza Elisabeti anali wouma, ndipo onse awiri anakalamba.

8 Ndipo panali, pakucita iye nchito yakupereka nsembe m'dongosolo la gulu lace, pamaso pa Mulungu, monga mwa macitidwe a kupereka nsembe,

9 adamgwera maere akufukiza zonunkhira polowa iye m'Kacisi wa Ambuye.

10 Ndipo khamu lonse la anthu Iinalikupemphera kunja nthawi ya zonunkhira.

11 Ndipo anamuonekera iye mngelo wa Ambuye, naimirira ku dzanja lamanja la guwa la nsembe la zonunkhira.

12 Ndipo Zakariya anadabwa pamene anamuona, ndipo mantha anamgwira.

13 Koma mngelo anati kwa iye, Usaope Zakariya, cifukwa kuti lamveka pemphero lako, ndipo mkazi wako adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamucha dzina lace Yohane.

14 Ndipo udzakhala nako kukondwera ndi msangalalo; ndipo anthu ambiri adzakondwera pa kubadwa kwace.

15 Pakuti iye adzakhala wamkuru pamaso pa Ambuye, ndipo sadzamwa konse vinyo kapena, kacasu; nadzadzazidwa ndi Mzimu Woyera, kuyambira asanabadwe.

16 Ndipo iye adzatembenuzira ana a Israyeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wao.

17 Ndipo adzamtsogolera iye, ndi mzimu ndi mphamvu ya Eliya, kutembenuzira mitima ya atate kwa ana ao, ndi osamvera kuti atsate nzeru ya olungama mtima; kukonzeratu Ambuye anthu okonzeka.

18 Ndipo Zakariya anati kwa mngelo, Ndidzadziwitsa ici ndi ciani? Pakuti ndine nkhalamba, ndipo zaka zace za mkazi wanga zacuruka.

19 Ndipo mngelo anayankha, nati kwa iye, ine ndine Gabrieli, woimirira pamaso pa Mulungu; ndipo ndinatumidwa kwa iwe kudzalankhula nawe, ndi kuuza iwe uthenga uwu wabwino.

20 Ndipo taona, udzakhala wotonthola ndi wosakhoza kulankhula, kufikira tsiku limene zidzacitika izi, popeza kuti sunakhulupirira mau, anga, amene adzakwanitsidwa pa nyengo yace.

21 Ndipo anthu analikulindira Zakariya, nazizwa ndi kucedwa kwace m'kacisimo.

22 Koma m'mene iye anaturukamo, sanatha kulankhula nao; ndipo anazindikira kuti iye adaona masomphenya m'Kacisimo. Ndipo iye analinkukodola iwo, nakhalabe wosalankhula.

23 Ndipo kunali, pamene masiku a utumiki wace anamarizidwa, anamuka kunyumba kwace.

24 Ndipo atatha masiku awa, Elisabeti mkazi wace anaima; nadzibisa miyezi isanu, nati,

25 Ambuye wandicitira cotero m'masiku omwe iye anandipenyera, kucotsa manyazi anga pakati pa anthu.

26 Ndipo mwezi wacisanu ndi cimodzi mngelo Gabrieli anatumidwa ndi Mulungu kunka ku mudzi wa ku Galileya dzina lace N azarete,

27 kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi mwamuna, dzina lace Yosefe, wa pfuko la Davine; ndipo dzina lace la namwaliyo ndilo Mariya.

28 Ndipo pakulowa mngelo anati kwa iye, Tikuoneni, wocitidwa cisomo, Ambuye ali ndi iwe.

29 Koma iye ananthunthumira ndi mau awa, nasinkhasinkha kulankhula uku nkutani.

30 Ndipo mngelo anati kwa iye, Usaope, Mariya; pakuti wapeza cisomo ndi Mulungu.

31 Ndipo taona, udzakhala ndi pakati, nudzabala mwana wamwamuna, nudzamucha dzina lace Yesu.

32 Iye adzakhala wamkuru, nadzachedwa Mwana wa Wamkurukuru: ndipo Ambuye Mulungu adzampatsa iye mpando wacifumu wa Davine atate wace:

33 ndipo iye adzacita ufumu pa banja la Yakobo ku nthawi zonse; ndipo ufumu wace sudzatha.

34 Koma Mariya anati kwa mngelo, ici cidzacitika bwanji, popeza ine sindidziwa mwamuna?

35 Ndipo mngelo anayankha, nati kwa iye, Mzimu Woyera adzafika pa iwe, ndi mphamvu ya Wamkulukulu idzakuphimba iwe: cifukwa cacenso Coyeraco cikadzabadwa, cidzachedwa Mwana wa Mulungu.

36 Ndipo taona, Elisabeti mbale wako, iyenso ali ndi pakati pa mwana wamwamuna m'ukalamba wace; ndipo mwezi uno uli wacisanu ndi cimodzi wa iye amene ananenedwa wouma.

37 Cifukwa 1 palibe mau amodzi akucokera kwa Mulungu adzakhala opanda mphamvu.

38 Ndipo Mariya anati, Onani, mdzakazi wa Ambuye; kukhale kwa ine monga mwa mau anu. Ndipo mngelo anacoka kwa iye.

39 Ndipo Mariya ananyamuka masiku amenewa, namuka ndi cangu ku dziko la mapiri ku mudzi wa Yuda;

40 nalowa m'nyumba ya Zakariya, nalankhula Elisabeti.

41 Ndipo panali pamene Elisabeti anamva kulankhula kwace kwa Mariya, mwana wosabadwayo anatsalima m'mimba mwace; ndipo Elisabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera;

42 nakweza mau ndi mpfuu waukuru, nati, 2 Wodalitsika iwe mwa akazi, ndipo codalitsika cipatso ca mimba yako,

43 Ndipo ici cicokera kuti kudza kwa ine, kuti adze kwa ine amace wa Ambuye wanga?

44 Pakuti ona, pamene mau a kulankhula kwako analowa m'makutu anga, mwana anatsalima ndi msangalalo m'mimba mwanga.

45 Ndipo wodala ali iye amene anakhulupirira; cifukwa zidzacitidwa zinthu zimene Ambuye analankhula naye.

46 3 Ndipo Mariya anati, Moyo wanga ulemekeza Ambuye,

47 Ndipo mzimu wanga wakondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.

48 Cifukwa iye anayang'anira umphawi wa mdzakazi wace; Pakuti taonani, kuyambira tsopano, anthu a mibadwo yonse adzandichula ine wodala.

49 Cifukwa iye Wamphamvuyo anandicitira ine zazikuru; 4 Ndipo dzina lace liri loyera.

50 5 Ndipo cifundo cace cifikira anthu a mibadwo mibadwo Pa iwo amene amuopa iye.

51 Iye anacita zamphamvu ndi mkono wace; 6 Iye anabalalitsa odzitama ndi mlingaliro wa mtima wao,

52 iye anatsitsa mafumu pa mipando yao yacifumu, Ndipo anakweza aumphawi,

53 7 Anawakhutitsa anjala ndi zinthu zabwino, Ndipo eni cuma anawacotsa opanda kanthu.

54 Anathangatira Israyeli mnyamata wace, Kuti akakumbukile cifundo,

55 8 (Monga analankhula kwa makolo athu) Kwa Abrahamu ndi kwa mbeu yace ku nthawi yonse.

56 Ndipo Mariya anakhala ndi iye ngati miyezi itatu, nabweranso kunyumba kwace.

57 Ndipo inakwanira nthawi ya Elisabeti, ya kubala kwace, ndipo anabala mwana wamwamuna.

58 Ndipo anansi ace ndi abale ace anamva kuti Ambuye anakulitsa cifundo cace pa iye; 9 nakondwera naye pamodzi.

59 Ndipo panali 10 tsiku lacisanu ndi citatu iwo anadza kudzadula kamwanako; ndipo akati amuche dzina la atate wace Zakariya.

60 Ndipo amace anayankha, kuti, lai; koma 11 adzachedwa Yohane.

61 Ndipo iwo anati kwa iye, Palibe wina wa abale ako amene achedwa dzina ili.

62 Ndipo anakodola atate wace, afuna amuche dzina liti?

63 Ndipo iye anafunsa colemberapo, nalemba, kuti, Dzina lace ndi Yohane. Ndipo anazizwa onse.

64 Ndipo 12 pomwepo panatseguka pakamwa pace, ndi lilume lace linamasuka, ndipo iye analankhula, nalemekeza Mulungu.

65 Ndipo panagwa mantha pa iwo onse akukhala oyandikana nao; ndipo analankhulalankhula nkhani izi zonse m'dziko: lonse la mapiri a Yudeya,

66 Ndipo onse amene anazimva anazisunga m'mtima mwao, nanena, Nangamwana uyu adzakhala wotani? Pakuti 13 dzanja la Ambuye linakhala pamodzi ndi iye.

67 Ndipo atate wace Zakariya anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nanenera za Mulungu, nati,

68 Wolemekezeka Ambuye, Mulungu wa Israyeli; 14 Cifukwa iye anayang'ana, nacitira anthu ace ciombolo,

69 Ndipo iye anatikwezera ife nyanga ya cipulumutso, Mwa pfuko la Davine mwana wace,

70 15 (Monga iye analankhula ndi m'kamwa mwa aneneri ace oyera mtima, a kale lomwe),

71 Cipulumutso ca adani athu, ndi pa dzanja la anthu onse amene atida ife;

72 16 Kucitira atate athu cifundo, Ndi kukumbukila pangano lace lopatulika;

73 Cilumbiro cimene iye anacilumbira kwa Abrahamu atate wathu,

74 Kutipatsa ife kuti titalanditsidwa ku dzanja la adani athu, 17 Tidzamtumikira iye, opanda mantha,

75 18 M'ciyero ndi cilungamo pamaso pace, masiku athu onse.

76 19 Eya, ndipo iwetu kamwanawe, udzanenedwa mneneri wa Wamkulukulu: 20 Pakuti udzatsogolera Ambuye, kukonza njira zace;

77 Kuwapatsa anthu ace adziwitse cipulumutso, 21 Ndi makhululukidwe a macimoao,

78 Cifukwa ca mtima wacifundo wa Mulungu wathu. M'menemo mbanda kuca wa kumwamba udzaticezera ife;

79 22 Kuwalitsira iwo okhala mumdima ndi mthunzi wa imfa; Kulunjikitsa mapazi athu mu njira ya mtendere.

80 Ndipo mwanayo anakula, nalimbika mu mzimu wace, ndipo 23 iye anali m'mapululu, kufikira masiku akudzionetsa yekha kwa Israyeli.

2

1 Ndipo kunali masiku aja, kuti lamulo linaturuka kwa Kaisara Augusto kuti dziko lonse lokhalamo anthu lilembedwe;

2 ndiko kulembera koyamba pokhala Kureniyo kazembe wa Suriya.

3 Ndipo onse anamuka kulembedwa, munthu ali yense ku mudzi wace.

4 Ndipo Yosefe yemwe anakwera kucokera ku Galileya, ku mudzi wa Nazarete, kunka ku Yudeya, ku mudzi wa Davine, dzina lace Betelehemu, cifukwa iye anali wa banja ndi pfuko lace la Davine;

5 kukalembedwa iye mwini pamodzi ndi Mariya, wopalidwa naye ubwenzi; ndi uyu anali ndi pakati,

6 Ndipo panali pokhaia iwo komweko, masiku ace a kubala anakwanira.

7 Ndipo iye anabala mwana wace wamwamuna woyamba; namkulunga iye m'nsaru, namgoneka modyera ng'ombe, cifukwa kuti anasowa malo m'nyumba ya alendo.

8 Ndipo panali abusa m'dziko lomwelo, okhala kubusa ndi kuyang'anira zoweta zao usiku.

9 Ndipo mngelo wa Ambuye anaimirira pa awo, ndi kuwala kwa Ambuye kunawaunikira kozungulira: ndipo anaopa ndi mantha akuru.

10 Ndipo mngelo anati kwa iwo, Musaope; pakuti onani, ndikuuzani inu uthenga wabwino wa cikondwero cacikuru, cimene cidzakhala kwa anthu onse;

11 pakuti wakubadwirani inu lero, m'mudzi wa Davide, Mpulumutsi, amene ali Kristu Ambuye.

12 Ndipo ici ndi cizindikilo kwa inu: Mudzapeza mwana wakhanda wokuta ndi nsaru atagonamodyera.

13 Ndipo dzidzidzi panali pamodzi ndi mngeloyo ambirimbiri a gulu la Kumwamba, natamanda Mulungu, nanena,

14 Ulemerero ukhale kwa Mulungu Kumwambamwamba, Ndi mtendere pansi pano mwa anthu amene akondwera nao.

15 Ndipo panali, pamene angelo anacokera kwa iwo kunka Kumwamba, abusa anati wina ndi mnzace, Tipitiretu ku Betelehemu, tikaone cinthu ici cidacitika, cimene Ambuye anatidziwitsira ife.

16 Ndipo iwo anadza ndi cangu, napeza Mariya, ndi Yosefe, ndi mwana wakhanda atagona modyera.

17 Ndipo iwo, m'mene anaona, anadziwitsa anthu za mau analankhulidwa kwa iwo a mwana uyu.

18 Ndipo anthu onse amene anamva anazizwa ndi zinthu abusa adalankhula nao.

19 Koma Mariya anasunga mau awa onse, nawalingalira mumtima mwace.

20 Ndipo abusawo anabwera, nalemekeza ndi kutamanda Mulungu pa zinthu zonse anazimva, naziona, monga kunalankhulidwa kwa iwo.

21 Ndipo pamene panakwanira masiku asanu ndi atatu akumdula iye, anamucha dzina lace Yesu, limene anachula mngeloyo asanalandiridwe iye m'mimba.

22 Ndipo pamene anakwanira masiku a kukonza kwao, monga mwa cilamulo ca Mose, iwo anakwera naye kunka ku Yerusalemu, kukamsonyeza iye kwa Ambuye,

23 (monga mwalembedwa m'cilamulo ca Ambuye, kuti mwamuna ali yense wotsegula pa mimba ya amace adzanenedwa wopatulika wa kwa Ambuye)

24 ndi kukapereka nsembe monga mwanenedwa m'citamulo ca Ambuye, njiwa ziwiri, kapena maunda awiri.

25 Ndipo onani, m'Yerusalemu munali munthu, dzina lace Simeoni; ndipo munthu uyu, wolungama mtima ndi wopemphera, analikulindira matonthozedwe a Israyeli; ndipo Mzimu Woyera anali pa iye.

26 Ndipo anamuululira Mzimu Woyera kuti sadzaona imfa, kufikira adzaona Kristu wace wa Ambuye.

27 Ndipo iye analowa kuKacisi ndi Mzimu: ndipo pamene atate ndi amace analowa ndi kamwanako Yesu, kudzamcitira iye mwambo wa cilamulo,

28 pomwepo iye anamlandira iye m'manja mwace, nalemekeza Mulungu, nati,

29 Tsopano, Ambuye, monga mwa mau anu aja, Lolani ine, kapolo wanu, ndicoke mumtendere;

30 Cifukwa maso anga adaona cipulumutso canu,

31 Cimene munakonza pamaso pa anthu onse,

32 Kuunika kukhale cibvumbulutso ca kwa anthu a mitundu, Ndi ulemerero wa anthu anu Israyeli.

33 Ndipo atate ndi amace anali kuzizwa ndi zinthu zolankhulidwa za iye.

34 Ndipo Simeoni anawadalitsa, nati kwa Mariya amace, Taona, Uyu waikidwa akhale kugwa ndi kunyamuka kwa anthu ambiri mwa. Israyeli; ndipo akhale cizindikilo cakutsutsana naco;

35 eya, ndipo lupanga lidzakupyoza iwe moyo wako; kuti maganizo a m'mitima yambiri akaululidwe.

36 Ndipo panali Anna, mneneri wamkazi, mwana wa Fanueli, wa pfuko la Aseri; amene anali wokalamba ndithu, nakhala ndi mwamuna wace, kuyambira pa unamwali wace,

37 zaka zisanu ndi ziwiri, ndipo anali wamasiye wa kufikira zaka zace: makumi asanu ndi atatu mphambu zinai, amene sanacoka kuKacisi, wotumikira Mulungu ndi kusala kudya ndi kupemphera usiku ndi usana.

38 Ndipo iye anafikako pa nthawi yomweyo, nabvomerezanso kutama Mulungu, nalankhula za iye kwa anthu onse 1 akuyembekeza ciombolo ca Yerusalemu.

39 Ndipo pamene iwo anatha zonse monga mwa cilamulo ca Ambuye, anabwera ku Galileya, ku mudzi kwao, ku Nazarete.

40 Ndipo 2 mwanayo anakula nalimbika, nalikudzala ndi nzeru; ndi cisomo ca Mulungu cinali pa iye.

41 Ndipo atate wace ndi amace 3 akamuka caka ndi caka ku Yerusalemu ku Paskha.

42 Ndipo pamene iye anakhala ndi zaka zace khumi ndi ziwiri, anakwera iwo monga macitidwe a phwando;

43 ndipo pakumariza masiku ace, pakubwera iw, mnyamatayo Yesu anatsala m'mbuyo ku Yerusalemu. Ndipo atate ndi amace sanadziwa;

44 koma iwo anayesa kuti iye ali m'cipiringu ca ulendo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi; ndipo anayamba kumfunafuna iye mwa abale ao ndi mwa anansi ao;

45 ndipo pamene sanampeza, anabwera ku Yerusalemu, namfunafuna iye.

46 Ndipo pakupita masiku atatu, anampeza iye m'Kacisi, analikukhala pakati pa aphunzitsi, namva iwo, nawafunsanso mafunso.

47 Ndipo 4 onse amene anamva iye anadabwa ndi cidziwitso cace, ndi mayankho ace.

48 Ndipo m'mene anamuona iye, anadabwa; ndipo amace anati kwa iye, Mwanawe, wacitiranji ife cotero; taona, atate wako ndi ine tinalikufunafuna Iwe ndi kuda nkhawa.

49 Ndipo iye anati kwa iwo, Kuli bwanji kuti munalikundifunafuna Ine? Simunadziwa kodi kuti kundiyenera Ine 5 ndikhale m'zace za Atate wanga?

50 Ndipo 6 sanadziwitsa mau amene iye analankhula nao.

51 Ndipo anatsika nao pamodzi nadza ku Nazarete; nawamvera iwo: ndipo 7 amace anasunga zinthu izi zonse mumtima mwace.

52 Ndipo Yesu 8 anakulabe m'nzeru ndi mumsinkhu, ndi m'cisomo ca pa Mulungu ndi ca pa anthu.

3

1 Ndipo pa caka cakhumi ndi cisanu ca ufumu wa Tiberiyo Kaisara, pokhala Pontiyo Pilato kazembe wa Yudeya, ndi Herode ciwanga ca Galileya, ndi Filipo mbale wace ciwanga ca dziko la Itureya ndi la Trakoniti, ndi Lusaniyo ciwanga ca Abilene;

2 pa ukuru wansembe wao wa Anasi ndi Kayafa, panadza mau a Mulungu kwa Yohane mwana wa Zakariya m'cipululu.

3 Ndipo iye anadza ku dziko lonse la m'mbali mwa Yordano, nalalikira ubatizo wa kulapa mtima kuloza ku cikhululukiro ca macimo;

4 monga mwalembedwa m'kalata wa mau a Yesaya mneneri, kuti, Mau a wopfuula m'cipululu, Konzani khwalala la Ambuye, Lungamitsani njira zace.

5 Cigwa ciri conse cidzadzazidwa, Ndipo phiri liri lonse ndi mtunda uti wonse zidzacepsedwa; Ndipo zokhota zidzakhala zolungama, Ndipo njira za zigoloondo zidzakhala zosalala;

6 Ndipo anthu onse adzaona cipulumutso ca Mulungu.

7 Cifukwa cace iye ananena kwa makamuwo a anthu amene anaturukira kukabatizidwa ndi iye, Obadwa a njoka inu, anakulangizani inu ndani kuthawa mkwiyo ulinkudza?

8 Cifukwa cace balani zipatso zakuyenera kulapa mtima, ndipo musayambe kunena mwa inu nokha, Atate wathu tiri naye ndiye Abrahamu: pakuti ndinena kwa inu, kuti ali ndi mphamvu Mulungu, mwa miyala iyi, kuukitsira Abrahamu ana.

9 Ndiponso tsopano lino nkhwangwa yaikidwa pa mizu ya mitengo; cotero mtengo uli wonse wosabala cipatso cabwino udulidwa, nuponyedwa pamoto.

10 Ndipo anthu a makamu anamfunsa iye, nanena, Ndipo tsono tizicita ciani?

11 Koma iye anayankha nanena kwa iwo, Iye amene ali nao malaya awiri apatse kwa iye amene alibe; ndi iye amene ali nazo zakudya acite comweco.

12 Ndipo amisonkho omwe anadza kudzabatizidwa, nati kwa iye, Mphunzitsi, ife tizicita ciani?

13 Koma iye anati kwa iwo, Musakapambe kanthu konse kakuposa cimene anakulamulirani.

14 Ndipo asilikari omwe anamfunsa iye, nati, Nanga ife tizicita ciani? Ndipo iye anati kwa iwo, Musaopse, musanamize munthu ali yense; khalani okhuta ndi kulipira kwanu.

15 Ndipo pamene anthu anali kuyembekezera, ndipo onse anaganizaganiza m'mitima yao za Yohane, ngati kapena iye ali Kristu;

16 Yohane anayankha, nanena kwa onse, Inetu ndikubatizani inu ndi madzi; koma wakundiposa ine mphamvu alinkudza, amene sindiyenera kumasula lamba la nsapato zace; Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto:

17 amene couluzira cace ciri m'dzanja lace, kuti ayeretse padwale pace, ndi kusonkhanitsa tirigu m'ciruli cace; koma mankhusu adzatentha m'moto wosazima.

18 Coteretu iye anauza anthu Uthenga Wabwino ndi kuwadandaulira zinthu zina zambiri.

19 Koma Herode mfumu ija, m'mene Yohane anamdzudzula cifukwa ca Herodiya, mkazi wa mbale wace, ndi ca zinthu zonse zoina Herode anazicita,

20 anaonjeza pa zonsezi icinso, kuti anatsekera Yohane m'nyumba yandende.

21 Ndipo panali pamene anthu onse anabatizidwa, ndipo Yesu anabatizidwa, nalikupemphera, kuti panatseguka pathambo,

22 ndipo Mzimu Woyera anatsika ndi maonekedwe a thupi lace ngati nkhunda, nadza pa iye; ndipo munaturuka mau m'thambo, kuti, Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa, mwa Iwe ndikondwera.

23 Ndipo Yesuyo, pamene anayamba nchito yace, anali monga wa zaka makumi atatu, ndiye (monga anthu adamuyesa) mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,

24 mwana wa Matati, mwana wa Levi, mwana wa Melki, mwana wa Yanai, mwana wa Yosefe,

25 mwana wa Matatio, mwana wa Amosi, mwana wa Naumi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,

26 mwana wa Maati, mwana wa Matatio, mwana wa Semeini, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda,

27 mwana wa Yoanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,

28 mwana wa Melki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, rrrvana wa Ere,

29 mwana wa Jose, mwana wa Eliezere, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,

30 mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliyakimu,

31 mwana wa Melea, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natanu, mwana wa Davine,

32 mwana wa Jese, mwana wa Obede, mwana wa Boazi, mwana wa Salmoni, mwana wa Naasoni,

33 mwana wa Aminadabu, mwana wa Ami, mwana wa Ezronu, mwana wa Farese, mwana wa Yuda,

34 mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,

35 mwana wa Seruki, mwana wa Reu, mwana wa Pelege, mwana wa Ebere, mwana wa Sala,

36 mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameke,

37 mwana wa Metusela, mwana wa Enoke, mwana wa Yaredi, mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,

38 mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.

4

1 Ndipo Yesu, wodzala ndi Mzimu Woyera, anabwera kucokera ku Yordano, natsogozedwa ndi Mzimu kunka kucipululu kukayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anai.

2 Ndipo iye sanadya kanthu masiku awo; ndipo pamene anatha anamva njala.

3 Ndipo mdierekezi anati kwa iye, Ngati muli Mwana wa Mulungu, uzani mwala uwu usanduke mkate.

4 Ndipo Yesu anayankha nati kwa iye, Kwalembedwa, kuti, Munthu sadzakhala ndi moyo ndi mkate wokha.

5 Ndipo m'mene anamtsogolera anakwera naye, namuonetsa iye maufumu onse a dziko lokhalamo anthu, m'kamphindi kakang'ono.

6 Ndipo mdierekezi anati kwa iye, Ine ndidzapatsa Inu ulamuliro wonse umenewu ndi ulemerero wao: cifukwa unaperekedwa kwa ine; ndipo ndiupatsa kwa iye amene ndifuna.

7 Cifukwa cace ngati Inu mudzagwadira pamaso panga, wonsewo udzakhala wanu.

8 Ndipo Yesu anayankha, nati kwa iye, Kwalembedwa, kuti, Ambuye Mulungu wako uzimgwadira, Ndipo iye yekha yekha uzimtumikira,

9 Ndipo anamtsogolera iye ku Yerusalemu, namuika iye pamwamba pa cimbudzi ca Kacisiyo, nati kwa iye, Ngati muli Mwana wa Mulungu, tadzigwetsani nokha pansi;

10 pakuti kwalembedwa, kuti, Adzalamulira angelo ace za, iwe, kuti akucinjirize,

11 Ndipo, Pa manja ao adzakunyamula iwe, Kuti ungagunde konse phazi lako pamwala,

12 Ndipo Yesu anayankha, nati kwa iye, Kwanenedwa, Usamuyese Ambuye Mulungu wako,

13 Ndipo mdierekezi, m'mene adamariza mayesero onse, analekana naye kufikira nthawi yina.

14 Ndipo Yesu anabwera ndi mphamvu ya Mzimu ku Galileya; ndipo mbiri yace ya iye inabuka ku dziko lonse loyandikira.

15 Ndipo iye anaphunzitsa m'masunagoge mwao, nalemekezedwa ndi anthu onse.

16 Ndipo anadza ku Nazarete, kumene analeredwa; ndipo tsiku la Sabata analowa m'sunagoge, monga anazolowera, naimiriramo kuwerenga m'kalata.

17 Ndipo anapereka kwa iye buku la Yesaya mneneri. Ndipo m'mene iye adafunyulula bukulo, anapeza pomwe panalembedwa,

18 Mzimu wa Ambuye uli paine, Cifukwa cace iye anandidzoza Ine ndiuze anthu osauka Uthenga Wabwino: Anandituma Ine kulalikira am'nsinga mamasulidwe, Ndi akhungu kuti apenyenso, Kuturutsa ndi ufuru ophwanyika,

19 Kulalikira caka cosankhika ca Ambuye.

20 Ndipo m'mene iye anapinda bukulo, nalipereka kwa mnyamata, anakhala pansi; ndipo maso ao a anthu onse m'sunagogemo anamyang'anitsa iye.

21 Ndipo anayamba kunena kwa iwo, kuti, Lero lembo ili lakwanitsidwa m'makutu anu.

22 Ndipo onse anamcitira iye umboni nazizwa ndi mau a cisomo akuturuka m'kamwa mwace; nanena, Kodi uyu si mwana wa Yosefe?

23 Ndipo anati kwa iwo, Kwenikweni mudzati kwa Ine nkhani iyi, Sing'anga iwe, tadziciritsa wekha: zonse zija tazimva zinacitidwa ku Kapernao, muzicitenso zomwezo kwanu kuno.

24 Ndipo iye anati, Indetu, ndinena kwa inu, kuti, Palibe mneneri alandirika ku dziko la kwao.

25 Koma zoonadi ndinena kwa inu, kuti, Munali akazi amasiye ambiri m'lsrayeli masiku ace a Eliya, pamene kunatsekedwa kumwamba zaka zitatu ndi miyezi isanu ndi umodzi, pamene panakhala njala yaikuru pa dziko lonselo;

26 ndipo Eliya sanatumidwa kwa mmodzi wa iwo, koma ku Sarepta wa ku Sidoniya, kwa mkazi wamasiye.

27 Ndipo munali akhate ambiri m'Israyeli masiku a Elisa mneneri; ndipo palibe mmodzi wa iwo anakonzedwa, koma Namani yekha wa ku Suriya.

28 Ndipo onse a m'sunagogemo anadzala ndi mkwiyo pakumva izi;

29 nanyamuka na mturutsira Iye kunja kwa mudziwo, nanka naye pamutu pa phiri pamene panamangidwa mudzi wao, kuti akamponye iye pansi.

30 Koma iye anapyola pakati pao, nacokapo.

31 Ndipo iye anatsika nadza ku Kapernao, ndiwo mudzi wa ku Galileya, Ndipo analikuwaphunzitsa iwo pa Sabata; ndipo anadabwa ndi ciphunzitso cace;

32 cifukwa mau ace anali ndi ulamuliro.

33 Ndipo munali m'sunagoge munthu, wokhala naco ciwanda conyansa; napfuula ndi mau olimba, kuti,

34 Ha! tiri ndi ciani ndi Inu, Yesu wa ku N azarete? kodi munadza kutiononga ife? ndikudziwani Inu muli yani, ndinu Woyera wace wa Mulungu.

35 Ndipo Yesu anamdzudzula iye, nanena, Tonthola, nuturuke mwa iye. Ndipo ciwandaco m'mene cinamgwetsa iye pakati, cinaturuka mwa iye cosampweteka konse.

36 Ndipo anthu onse anadabwa, nalankhulana wina ndi mnzace, nanena, Mau amenewa ali otani? cifukwa ndi ulamuliro ndi mphamvu angolamulira mizimu yonyansa, ndipo ingoturuka.

37 Ndipo mbiri yace ya iye inafalikira ku malo onse a dziko Ioyandikira.

38 Ndipo iye ananyamuka kucokera m'sunagoge, nalowa m'nyumba ya Simoni. Koma momwemo munali mpongozi wace wa Simoni, anagwidwa ndi nthenda yolimba yamalungo; ndipo anampempha Yesu za iye.

39 Ndipo iye anaimirira, naweramira pa iye, nadzudzula nthendayo; ndipo inamleka iye: ndipo anauka msangatu, nawatumikira.

40 Ndipo pakulowa dzuwa anthu onse amene anali nao odwala ndi nthenda za mitundu mitundu, anadza nao kwa iye; ndipo iye anaika manja ace pa munthu ali yense wa iwo, nawaciritsa.

41 Ndi ziwanda zomwe zinaturuka mwa ambiri, ndi kupfuula, kuti, Inu ndinu Mwana wa Mulungu. Ndipo iye anazidzudzula, wosazilola kulankhula, cifukwa zinamdziwa kuti iye ndiye Kristu.

42 Ndipo kutaca anaturuka iye nanka ku malo acipululu; ndi makamu a anthu analikwnfunafuna iye, nadza nafika kwa iye, nayesa kumletsa iye, kuti asawacokere.

43 Koma anati kwa iwo, Kundiyenera Ine ndilalikire Uthenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu ku midzi yinanso: cifukwa ndinatumidwa kudzatero.

44 Ndipo iye analikulalikira m'masunagoge a ku Galileya.

5

1 Ndipo panali, pakumkanikiza khamu la anthu, kudzamva mau a Mulungu, iye analikuimirira m'mbali mwa nyanja ya Genesarete;

2 ndipo anaona ngalawa ziwiri zinakhala m'mbali mwa nyanja; koma asodzi a nsomba adaturuka m'menemo, nalikutsuka makoka ao.

3 Ndipo iye analowa m'ngalawa imodzi, ndiyo yace ya Simoni, nampempha iye akankhe pang'ono. Ndipo anakhala pansi m'menemo, naphunzitsa m'ngalawa makamuwo a anthu.

4 Ndipo pamene iye analeka kulankhula, anati kwa Simoni, Kankhira kwa kuya, nimuponye makoka anu kukasodza.

5 Ndipo Simoni anayankha, nati, Ambuye, tinagwiritsa nchito usiku wonse osakola kanthu, koma pa mau anu ndidzaponya makoka.

6 Ndipo pamene anacita ici, anazinga unyinji waukuru wansomba; ndipo makoka ao analinkung'ambika;

7 ndipo anakodola anzao a m'ngalawa yinayo, adze awathangate. Ndipo anadza, nadzaza ngalawa zonse ziwiri, motero kuti zinalinkumira.

8 Koma Simoni Petro, pamene anaona, anagwa pansi pa mabondo ace a Yesu, nanena, Mucoke kwa ine, Ambuye, cifukwa ndine munthu wocimwa.

9 Pakuti cizizwo cidagwira iye, ndi onse amene anali naye, pa kusodzako kwa nsomba zimene anazikola;

10 ndipo cimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, amene anali anzace a Simoni. Ndipo Yesu anati kwa Simoni, Usaope, kuyambira tsopano udzakhala msodzi wa anthu.

11 Ndipo m'mene iwo anakoceza ngalawa zao pamtunda, anasiya zonse, namtsata iye.

12 Ndipo panali, pamene iye anali m'mudzi wina, taona, munthu wodzala ndikhate; ndipopameneanaona Yesu, anagwa nkhope yace pansi, nampempha iye, nanena, Ambuye, ngati mufuna mungathe kundikonza.

13 Ndipo iye anatambalitsa dzanja lace, namkhudza, nanena, Ndifuna, takonzeka, Ndipo pomwepo khate linacoka kwa iye.

14 Ndipo iye anamuuzitsa, kuti asanene kwa munthu ali yense; koma ucoke, nudzionetse wekha kwa wansembe, nupereke nsembe ya pa cikonzedwe cako, monga adalamulira Mose, kukhale umboni kwa iwo.

15 Koma makamaka mbiri yace ya iye inabuka: ndipo mipingo yambiri ya anthu inasonkhanakudzamvera, ndi kudzaciritsidwa nthenda zao.

16 Koma iye anazemba, nanka m'mapululu, nalikupemphera.

17 Ndipo panali tsiku limodzi la masiku awo, iye analikuphunzitsa; ndipo analikukhalapo Afarisi ndi aphunzitsi a malamulo, amene anacokera ku midzi yonse ya ku Galileya, ndi Yudeya ndi Yerusalemu: ndipo mphamvu ya Ambuye inali ndi iye yakuwaciritsa,

18 Ndipo onani, anthu alikunyamulira pakama munthu wamanjenje; nafunafuna kulowa naye, ndi kumuika pamaso pa iye.

19 Ndipo posapeza polowa naye, cifukwa ca unyinji wa anthu, anakwera pamwamba pa chindwi, namtsitsira iye poboola pa chindwi ndi kama wace, namfikitsa pakati pomwe pamaso pa Yesu.

20 Ndipo iye, pakuona cikhulupiriro cao, anati, Munthu iwe, macimo ako akhululukidwa.

21 Ndipo alembi ndi Afarisi anayamba kuyesayesa mumtima mwao, kuti, ndani Uyu alankhula zomcitira Mulungu mwano? Ndani angathe kukhululukira macimo, koma Mulungu yekha?

22 Koma Yesu anadziwa zoyesayesa zao, nayankha, nati kwa iwo, Muyesayesa bwanji m'mitima yanu?

23 Capafupi nciti, kunena, Akhululukidwa kwa iwe macimo ako; kapena kunena, Tauka, nuyende?

24 Koma kuti mudziwe kuti Mwana wa munthu ali nayo mphamvu pa dziko lapansi yakukhululukira macimo, (anati iye kwa wamanjenjeyo), Ndinena kwa iwe, Tauka, nusenze kama wako, numuke kunyumba kwako.

25 Ndipo pomwepo anaimirira pamaso pao, nasenza cimene adagonapo, nacokapo, kunka kunyumba kwace, wakulemekeza Mulungu.

26 Ndipo cizizwo cinagwira anthu onse, ndipo analemekeza Mulungu nadzazidwa ndi mantha, nanena kuti, Lero taona zodabwitsa.

27 Ndipo zitatha izi iye anaturuka, Danna munthu wamsonkho, dzina lace Levi, alikukhala polandira msonkho, nati kwa iye, Unditsate Ine.

28 Ndipo iye anasiya zonse, nanyamuka, namtsata iye.

29 Ndipo Levi anamkonzera iye phwando lalikuru kunyumba kwace; ndipo panali khamu lalikuru la amisonkho, ndi enanso amene analikuseama pacakudya pamodzi nao.

30 Ndipo Afarisi ndi alembi ao anang'ung'udza kwa ophunzira ace nanena, kuti, Bwanji inu mukudya ndi kumwa pamodzi ndi anthu amisonkho ndi ocimwa?

31 Ndipo Yesu anayankha, nati kwa iwo, Amene ali olimba safuna sing'anga; koma akudwala ndiwo.

32 Sindinadza Ine kuitana olungama, koma ocimwa kuti atembenuke mtima,

33 Ndipo iwo anati kwa iye, Ophunzira a Yohane amasala kudya kawiri kawiri, ndi kucita mapemphero; cimodzimodzinso iwo a Afarisi; koma anu amangokudya ndi kumwa.

34 Koma Yesu anati kwa iwo, Kodi mungathe kuletsa anyamata a ukwati asadye, pamene mkwati ali nao pamodzi?

35 Koma masiku adzafika; ndipo pamene mkwati adzacotsedwa kwa iwo, pamenepo adzasala kudya masiku omwewo.

36 Ndipo iye ananenanso fanizo kwa iwo, kuti, Palibe munthu ang'amba cigamba ca maraya arsopano, naciphatika pa maraya akale; cifukwa ngati atero, angong'ambitsa atsopanowo, ndi cigamba ca atsopanowo sicidzayenerana ndi akalewo.

37 Ndipo palibe munthu atsanulira vinyo watsopano m'matumba akale; cifukwa ngati atero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa matumba, ndipo ameneyo adzatayika, ndi matumba adzaonongeka.

38 Koma kuyenera kutsanulira vinyo watsopano m'matumba atsopano.

39 Ndipo palibe munthu atamwa vinyo wakale afuna watsopano; pakuti anena, Wakale ali wokoma.

6

1 Ndipo kunali tsiku la Sabata, iye analinkupita pakati pa minda ya tirigu; ndipo ophunzira ace analinkubudula ngala za tirigu, nazifikisa m'manja mwao, nadya.

2 Koma Afarisi ena anati, Mucitiranji cosaloledwa kucitika tsiku la Sabata?

3 Ndipo Yesu anayankha nati kwa iwo, Kodi simunawerenganso ngakhale cimene anacita Davine, pamene paja anamva Njala, iye ndi iwo anali naye pamodzi,

4 kuti analowa m'nyumba ya Mulungu, natenga mikate yoonetsera, nadya, napatsanso iwo anali naye pamodzi; imeneyi yosaloledwa kudya ena koma ansembe okha?

5 Ndipo iye ananena kwa iwo, kuti, Mwana wa munthu ali Mbuye wa tsiku la Sabata.

6 Ndipo kunali tsiku lina la Sabata, iye analowa m'sunagoge naphunzitsa. Ndipo munali munthu momwemo, ndipo dzanja lace lamanja linali lopuwala.

7 Ndipo alembi ndi Afarisi analikumzonda iye, ngati adzaciritsa tsiku la Sabata; kuti akapeze comneneza iye.

8 Koma iye anadziwa maganizo ao; nati kwa munthuyo wa dzanja lace lopuwala, Nyamuka, nuimirire pakatipo.

9 Ndipo Iyeananyamuka, naimirira. Ndipo Yesuanati kwa iwo, Ndikufunsani inu, Kodi nkulola tsiku la Sabata, kucita zabwino, kapena kucita zoipa? kupulumutsa moyo, kapena kuuononga?

10 Ndipo pamene anaunguza-unguza pa iwo onse, anati kwa iye, Tansa dzanja lako, Ndipo iye anatero, ndi dzanja lace lina; bwerera momwe.

11 Koma iwowo anagwidwa misala; nalankhulana wina ndi mnzace kuti amcitire Yesu ciani.

12 Ndipo kunali masiku awa, iye anaturuka nanka kuphiri kukapemphera; nacezera usiku wonse m'kupemphera kwa Mulungu.

13 Ndipo kutaca, anaitana ophunzira ace; nasankha mwa iwo khumi ndi awiri, amene anawachanso dzina lao atumwi:

14 Simoni, amene anamuchanso Petro, ndi Andreya mbale wace, ndi Yakobo, ndi Yohane, ndi Filipo, ndi Bartolomeyo,

15 ndi Mateyu, ndi Tomasi, ndi Yakobo mwana wa Alifeyo, ndi Simoni wochedwa Zelote,

16 ndi Yuda mwana wa Yakobo, ndi Yudase Isikariote, amene anali wompereka iye.

17 Ndipo iye anatsika nao, naima pacidikha, ndi khamu lalikuru la ophunzira ace, nw unyinji waukuru wa anthu a ku Yudeya lonse ndi Yerusalemu, ndi a ku mbali ya nyanja ya ku Turo ndi Sidoni, amene anadza kudzamva iye ndi kudzaciritsidwa nthenda zao;

18 ndipo obvutidwa ndi mizimu yonyansa anaciritsidwa,

19 ndi khamu lonse lija linafuna kumkhudza iye; cifukwa munaturuka mphamvu mwa iye, niciritsa onsewa.

20 Ndipo iye anakweza maso ace kwa ophunzira ace, nanena, Odala osauka inu; cifukwa uli wanu ufumu wa Mulungu.

21 Odala inu akumva njala tsopano; cifukwa mudzakhuta. Odala inu akulira tsopano; cifukwa mudzaseka.

22 Odala inu, pamene anthu adzada inu, nadzapatula inu, nadzatonza inu, nadzalitaya dzina lanu monga loipa, cifukwa ca Mwana wa munthu.

23 Kondwerani tsiku lomweli, tumphani ndi cimwemwe; pakuti onani, mphotho zanu nzazikuru Kumwamba; pakuti makolo ao anawacitira aneneri zonga zomwezo.

24 Koma tsoka inu eni cuma! cifukwa mwalandira cisangalatso canu.

25 Tsoka inu okhuta tsopano! cifukwa mudzamva njala, Tsoka inu, akuseka tsopano! cifukwa mudzacita maliro ndi kulira misozi.

26 Tsoka inu, pamene anthu onse adzanenera inu zabwino! pakuti makolo ao anawatero momwemo ananeri onama.

27 Koma ndinena kwa inu akumva, Kondanani nao adani anu; citirani zabwino iwo akuda inu,

28 dalitsani iwo akutemberera inu, pemphererani iwo akucitira inu cipongwe.

29 Iye amene akupanda iwe pa tsaya limodzi umpatsenso linzace; ndi iye amene alanda copfunda cako, usamkanize malaya ako.

30 Munthu ali yense akakupempha kanthu, umpatse; ndi iye amene alanda zako, usazipemphanso.

31 Ndipo monga mufuna inu kuti anthu adzakucitirani inu, muwacitire iwo motero inu momwe.

32 Ndipo 1 ngati muwakonda iwo akukondana ndinu, mudzalandira ciyamiko cotani? pakuti ocimwa omwe akonda iwo akukondana nao.

33 Ndipo ngati muwacitira zabwino iwo amene akucitirani, inu zabwino, mudzalandira ciyamiko cotani? pakuti anthu ocimwa omwe amacita comweco.

34 Ndipo 2 ngati mukongoletsa kanthu kwa iwo amene muyembekeza kulandiranso, mudzalandira ciyamiko cotani? pakuti inde anthu ocimwa amakongoletsa kwa ocimwa anzao, kuti alandirenso momwemo.

35 Koma 3 takondanani nao adani anu, ndi kuwacitira zabwino, ndipo kongoletsani osayembekeza kanthu konse, ndipo mphotho yanu idzakhala yaikuru, ndipo 4 inu mudzakhala ana a Wamkurukuruyo; cifukwa iye acitira zokoma anthu osayamika ndi oipa.

36 Khalani inu acifundo monga Atate wanu ali wacifundo. Ndipo musamaweruza, ndipo simudzaweruzidwa.

37 Ndipo 5 musawatsutsa, ndipo simudzatsutsidwa. Masulani, ndipo mudzamasulidwa.

38 6 Patsani, ndipo kudzapatsidwa kwa inu; muyeso wabwino, wotsendereka, wokucumuka, wosefukira, anthu adzakupatsani m'manja mwanu. Pakuti 7 kudzayesedwa kwa inu ndi muyeso womwewo muyesa nao inu.

39 Ndipo iye ananenanso nao fanizo, 8 Kodi munthu wakhungu angathe kutsogolera mnzace wakhungu? kodi sadzagwa onse awiri m'mbuna?

40 9 Wophunzira saposa mphunzitsi wace; koma yense, m'mene atakonzedwa mtima, adzafanana ndi mphunzitsi wace.

41 Ndipo uyang'aniranji kacitsotso kali m'diso la mbale wako, koma mtanda wa m'diso la iwe mwini suuzindikira?

42 10 Kapena ungathe bwanji kunena kwa mbale wako, Mbale iwe, leka ndicotse kacitsotso kali m'diso lako, wosayang'anira iwe mwini mtanda uli m'diso lako? Wonyenga iwe! thanga wacotsa mtandawo m'diso lako, ndipo pomwepo udzayang'anitsa bwino kucotsa kacitsotso ka m'diso la mbale wako.

43 Pakuti 11 palibe mtengo wabwino wakupatsa zipatso zobvunda; kapenanso mtengo woipa wakupatsa zipatso zabwino,

44 Pakuti 12 mtengo uli wonse uzindikirika ndi cipatso cace. Pakuti anthu samachera nkhuyu paminga, kapena pamtungwi samachera mphesa,

45 13 Munthu wabwino aturutsa zabwino m'cuma cokoma ca mtima wace; ndi munthu woipa aturutsa zoipa m'coipa cace: pakuti m'kamwa mwace mungolankhula mwa kucuruka kwa mtima wace.

46 Ndipo 14 mundichuliranji Ine, Ambuye, Ambuye, ndi kusacita zimene ndizinena?

47 15 Munthu ali yense wakudza kwa Ine, ndi kumva mau anga, ndi kuwacita, ndidzakusonyezani amene afanana naye.

48 Iye afanafana ndi munthu wakumanga nyumba, amene anakumba pansi ndithu, namanga maziko a nyumbayo pathanthwe; ndipo pamene panadza cigumula, mtsinje unagunda pa nyumbayo, ndipo sunakhoza kuigwedeza; cifukwa idamangika bwino.

49 Koma iye amene akumva, ndi kusacita, afanafana ndi munthu wakumanga nyumba pa nthaka yopanda maziko; pa imeneyo unagunda mtsinje, ndipo inagwa pomwepo; ndipo kugumuka kwace kwa nyumbayo kunali kwakukuru.

7

1 Pamene Yesu adamariza mau ace onse m'makutu a anthu, analowa m'Kapernao.

2 Ndipo kapolo wa kenturiyo, wokondedwa naye, anadwala, nafuna kutsirizika.

3 Ndipo pamene iye ana-I mva za Yesu, anatuma kwa iye akuru a Ayuda, namfunsa iye kuti adze kupulumutsa kapolo wace.

4 Ndipo iwo, pakufika kwa Yesu, anampempha iye koumirira, nati, Ayenera iye kuti mumcitire ici;

5 pakuti akonda mtundu wathu, ndipo anatimangira ife sunagoge.

6 Ndipo Yesu anapita nao. Ndipo pakufika iye tsono pafupi panyumba yace, kenturiyo anatuma kwa iye abwenzi ace, kunena naye, Ambuye, musadzibvute; pakuti sindiyenera ine kuti mudzalowe pansi pa chindwi langa;

7 cifukwa cace ine sindinadziyesera ndekha woyenera kudza kwa Inu: koma nenani mau, ndipo mnyamata wanga adzaciritsidwa.

8 Pakuti inenso ndiri munthu wakumvera akuru anga, ndiri nao asilikari akumvera ine: ndipo ndinena kwa uyu, Muka, namuka; ndi kwa wina, Idza, nadza; ndipo kwa kapolo wanga Tacita ici, nacita.

9 Koma Yesu pakumva zimenezo anazizwa naye, napotolokera kwa anthu a mpingo wakumtsata iye, nati, Ndinena kwa inu, sindinapeza, ngakhale mwa Israyeli, cikhulupiriro cacikuru cotere.

10 Ndipo pakubwera ku nyumba otumidwawo, anapeza kapoloyo wacira ndithu.

11 Ndipo kunali, katapita kamphindi, iye ana pita kumudzi, dzina lace Nayini; ndipo ophunzira ace ndi mpingo waukuru wa anthu anapita nave.

12 Ndipo pamene anayandikira ku cipata ca mudziwo, onani, anthu analikunyamula munthu wakufa, mwana wamwamuna mmodzi yekha, amace ndiye mkazi wamasiye; ndipo anthu ambiri a kumudzi anali pamodzi naye.

13 Ndipo pamene Ambuye anamuona, anagwidwa ndi cifundo cifukwa ca iye, nanena naye, Usalire.

14 Ndipo anayandikira, nakhudza cithatha; ndipo akumnyamulawo anaima. Ndipo iye anati, Mnyamata iwe, ndinena ndi iwe, Tauka.

15 Ndipo wakufayo anakhala tsonga, nayamba kulankhula. Ndipo anampereka kwa amace.

16 Ndipo mantha anagwira onsewo: ndipo analemekeza Mulungu, nanena kuti, Mneneri wamkuru wauka mwa ife; ndipo Mulungu wadzaceza ndi anthu ace.

17 Ndipo mbiri yace imeneyo inabuka ku Yudeya lonse, ndi ku dziko lonse loyandikira.

18 Ndipo ophunzira a Yohane anamuuza iye zonsezi.

19 Ndipo Yohane anaitana awiri a ophunzira ace, nawatuma kwa Ambuye, nanena, Kodi ndinu wakudzayo, kapena tiyang'anire wina?

20 Ndipo pakufika kwa iye anthu awo, anati, Yohane Mbatizi watituma ife kwa Inu, kuti, Kodi ndinu wakudzayo, kapena tiyang'anire wina?

21 Nthawi yomweyo iye anaciritsa anthu ambiri nthenda zao, ndi zobvuta, ndi mizimu yoipa; napenyetsanso anthu akhungu ambiri.

22 Ndipo anayankha, nati kwa iwo, Mukani, muuze Yohane zimene mwaziona, nimwazimva; anthu akhungu alandira kuona kwao, opunduka miyendo ayenda, akhate akonzedwa, ogontha akumva, akufa aukitsidwa, kwa aumphawi ulalikidwa Uthenga Wabwino.

23 Ndipo wodala iye amene sakhomudwa cifukwa ca Ine.

24 Ndipo atacoka amithenga ace a Yohane, iye anayamba kunena za Yohane kwa anthu a makamu aja, nati, Munaturuka kunka kucipululu kukapenya ciani? Bango logwedezeka ndi mphepo kodi?

25 Koma munaturuka kukaona ciani? Munthu wobvala zobvala zofewa kodi? Onani, iwo akubvala zolemera, ndi akukhala odyerera, ali m'makuka a mafumu.

26 Koma munaturuka kukaona ciani? Mneneri kodi? Etu, ndinena kwa inu, ndipo wakuposa mneneri.

27 Uyu ndi iye amene kunalembedwa za iye, Ona, ndituma Ine mthenga wanga akutsogolere, Amene adzakukonzera njira yako pamaso pako.

28 Ndinena kwa inu, kuti, Mwa akubadwa ndi akazi palibe mmodzi wamkuru woposa Yohane; koma iye amene ali wamng'ono mu Ufumu wa Mulungu amposa iye.

29 Ndipo anthu onse ndi amisonkho omwe, pakumva, anabvomereza kuti Mulungu ali wolungama, popeza anabatizidwa iwo ndi ubatizo wa Yohane.

30 Koma Afarisi ndi acilamulo anakaniza uphungu wa Mulungu kwa iwo okha, popeza sanabatizidwa ndi iye.

31 Ndipo, ndidzafanizira ndi ciani anthu a mbadwo uno? ndipo afanana ndi ciani?

32 Angofanana ndi ana akukhala pamsika, ndi kuitanizana wina ndi mnzace, ndi kunena, Ife tinakulizirani citoliro, ndipo inu simunabvina ai; tinabuma maliro, ndimo simunalira ai.

33 Pakuti Yohane Mbatizi wafika wosadya mkate ndi wosamwa vinyo; ndipo munena, Ali ndi ciwanda.

34 Mwana wa munthu wafika wakudya ndi wakumwa; ndipo munena, Onani, munthu wosusuka ndi wakumwaimwa vinyo, bwenzi la amisonkho ndi anthu ocimwa!

35 Ndipo nzeru iyesedwa yolungama ndi ana ace onse.

36 Ndipo mmodzi wa Afarisi anamuitana iye kuti akadye naye. Ndipo analowa m'nyumba ya Mfarisi, naseama pacakudya.

37 Ndipo onani, mkazi wocimwa, amene anali m'mudzimo; ndipo pakudziwa kuti Yesu analikuseama pacakudya m'nyumba ya Mfarisi, anatenga nsupa yaalabastero ya mafuta onunkhira bwino,

38 naimirira kumbuyo, pa mapazi ace, nalira, nayamba kukhathamiza mapazi ace ndi misozi, nawapukuta ndi tsitsi la mutu wace, nampsompsonetsa mapazi ace, nawadzoza ndi mafuta onunkhira bwino.

39 Koma Mfarisi, amene adamuitana iye, pakuona, ananena mwa yekha, nati, Akadakhala mneneri uyu akadazindikira ali yani, ndi wotani mkaziyo womkhudza iye, cifukwa ali wocimwa.

40 Ndipo Yesu anayankha nati kwa iye, Simoni, ndiri ndi kanthu kakunena kwa iwe. Ndipo iye anabvomera, Mphunzitsi, nenani.

41 Munthu wokongoletsa ndalama anali nao amangawa awiri; mmodziyo anali ndi mangawa ace a marupiya mazana asanu, koma mnzace makumi asanu.

42 Popeza analibe cobwezera iwo, anawakhululukira onse awiri. Cotero, ndani wa iwo adzaposa kumkonda?

43 Simoni anayankha, nati, Ndiyesa kuti, iye amene anamkhululukira zoposa,

44 Ndipo anati kwa iye, Waweruza bwino. Ndipo m'mene iye anaceukira kwa mkaziyo, anati kwa Simoni, Upenya mkazi ameneyu kodi? Ndinalowa m'nyumba yako, sunandipatsa madzi akusambitsa mapazi anga; koma uyu anakonkha mapazi anga ndi misozi, nawapukuta ndi tsitsi lace.

45 Sunandipatsa mpsompsono wa cibwenzi; koma uyu sanaleka kupsompsonetsa mapazi anga, cilowere muno Ine.

46 Sunandidzoza mutu wanga ndi mafuta; koma nyu anadzoza mapazi anga ndimafuta onunkhira bwmo.

47 Cifukwa cace, ndinena kwa iwe, Macimo ace, ndiwo ambiri, akhululukidwa; cifukwa anakonda kwambiri; koma munthu amene anamkhululukira pang'ono, iye akonda pang'ono.

48 Ndipo anati kwa mkazi, Macimo ako akhululukidwa.

49 Ndipo iwo akuseama naye pacakudya anayamba kunena mwa okha, Uyu ndani amene akhululukiranso macimo?

50 Ndipo Iyeanati kwa mkaziyo, Cikhulupiriro cako cakupulumutsa iwe; muka ndi mtendere.

8

1 Ndipo kunali, katapita kamphindi anayendayenda kumizinda ndi kumidzi, kulalikira ndi kuwauza U thenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu, ndi pamodzi naye khumi ndi awiriwo,

2 ndi akazi ena amene anaciritsidwa mizimu yoipa ndi nthenda zao, ndiwo, Mariya wonenedwa Magadalene, amene ziwanda zisanu ndi ziwiri zinaturuka mwa iye,

3 ndi Yohana, mkazi wace wa Kuza kapitao wa Herode, ndi Susana, ndi ena ambiri, amene anawatumikira ndi eumacao.

4 Ndipo pamene khamu lalikuru la anthu linasonkhana, ndi anthu a ku midzi yonse anafika kwa iye, anati mwa fanizo:

5 Anaturuka wofesa kukafesa mbeu zace; ndipo m'kufesa kwace zina zinagwa m'mbali mwa njira; ndipo zinapondedwa, ndi mbalame za m'mlengalenga zinatha kuzidya.

6 Ndipo zina zinagwa pathanthwe; ndipo pakumera zinatofa msanga, cifukwa zinalibe mnyontho.

7 Ndipo zina zinagwa pakati pa minga; ndi mingayo inapuka pamodzi nazo, nizitsamwitsa.

8 Ndipo zina zinagwa pa nthaka yokoma, ndipo zinamera, ndi kupatsa zipatso zamakumikhumi. Pakunena iye izi anapfuula, iye amene ali ndi makutu akumva amve.

9 Ndipo ophunzira ace anamfunsa Iye, kuti, Fanizo ili liri lotani?

10 Ndipo iye anati, Kwapatsidwa kwa inu kuzindikira zinsinsi za Ufumu wa Mulungu; koma kwa ena otsala ndinena nao mwa mafanizo; kuti pakuona sangaone, ndi pakumva sangadziwitse,

11 Koma fanizoli litere: Mbeuzo ndizo mau a Mulungu,

12 Ndipo za m'mbali mwa njira ndiwo anthu amene adamva; pamenepo akudza mdierekezi, nacotsa mau m'mitima yao, kuti angakhulupirire ndi kupulumuka.

13 Ndipo za pathanthwe ndiwo amene, pakumva, alandira mau ndi kukondwera; koma alibe mizu; akhulupirira kanthawi, ndipo pa nthawi ya mayesedwe angopatuka.

14 Ndipo zija zinagwa ku mingazi, ndiwo amene adamva, ndipo m'kupita kwao atsamwitsidwa ndi nkhawa, ndi cuma, ndi zokondweretsa za moyo, ndipo sakhwimitsa zipatso zamphumphu.

15 Ndipo zija za m'nthaka yokoma, ndiwo amene anamva mau nawasunga mu mtima woona ndi wabwino, nabala zipatso ndi kupirira.

16 Ndipo palibe munthu, atayatsa, nyali, aibvundikira ndi cotengera, kapena kuiika pansi pa kama; koma aiika pacoikapo, kuti iwo akulowamo aone kuunikaku.

17 Pakuti palibe cinthu cobisika, cimene sicidzakhala coonekera; kapena cinsinsi cimene sicidzadziwika ndi kubvumbuluka.

18 Cifukwa cace yang'anirani mamvedwe anu; pakuti kudzapatsidwa kwa iye amene ali naco; ndipo kwa iye amene alibe cidzacotsedwa, cingakhale cija aoneka ngati ali naco.

19 Ndipo anadza kwa iye amace ndi abale ace, ndipo sanakhoza ku: mfika, cifukwa ca khamu la anthu.

20 Ndipo anamuuza iye, kuti, Amai wanu ndi abale anu alinkuima kunja, nafuna kuona Inu.

21 Koma iye anayankha, nati kwa iwo, Amai wanga ndi abale anga ndiwo amene akumva mau a Mulungu, nawacita.

22 Ndipo panali limodzi la masiku aja, iye analowa m'ngalawa, ndi ophunzira ace; nati kwa iwo, Tiolokere ku tsidya lija la nyanja; ndipo anakankhiramo.

23 Ndipo m'mene iwo anali kupita pamadzi, iye anagona tulo, Ndipo panyanja panatsikira namondwe wa mphepo; ndipo podzala ndi madzi, analimkuopsedwa.

24 Ndipo anadza kwa iye, namuutsa, nanena, Ambuye, Ambuye, titayika, Ndipo anauka, nadzudzula mphepo ndi mafunde ace a madzi; pomwepo zinaleka, ndipo panagwa batao

25 Ndipo iye anati kwa iwo, Cikhulupiriro canu ciri kuti? Ndipo m'kucita mantha anazizwa iwo, nanena wina ndi mnzace, Uyu ndani nanga, kuti angolamula mphepo ndi madzi, ndipo zimvera iye?

26 Ndipo iwo anakoceza kudooko ku dziko la Agerasa, ndilo Iopenyana ndi Galileya.

27 Ndipo ataturuka pamtanda iye, anakomana naye mwamuna wa kumudzi, amene anali nazo ziwanda; ndipo masiku ambiri sanabvala cobvala, nisanakhala m'nyumba, koma m'manda.

28 Ndipo pakuona Yesu, iye anapfuula, nagwa pansi pamaso pace, nati ndi mau akuru, Ndiri naco ciani ndi Inu, Yesu Mwana wa Mulungu Wamkurukuru? Ndikupemphani Inu musandizunze.

29 Pakuti iye adalamula mzimu wonyansa uturuke mwa munthuyo. Pakuti nthawi zambiri unamgwira; ndipo anthu anammanga ndi maunyolo ndi matangadza kumsungira; ndipo anamwetula zomangirazo, nathawitsidwa ndi ciwandaco kumapululu.

30 Ndipo Yesu anamfunsa iye, kuti, Dzina lako ndiwe yani? Ndipo anati, Legio, cifukwa ziwanda zambiri zidalowa mwa iye.

31 Ndipo zinampempha iye, kuti asazilamulire zicoke kulowa kuphompho.

32 Ndipo panali pamenepo gulu la nkhumba zambiri zirinkudya m'phiri. Ndipo zinampempha Iye kuti azilole zilowe mu izo. Ndipo anazilola.

33 Ndipo ziwandazo zinaturuka mwa munthu nizilowa mu nkhumba: ndipo gululo linatsika liwiro potsetsereka ndi kulowa m'nyanjamo, nilitsamwa.

34 Ndipo akuwetawo m'mene anaona cimene cinacitika, anathawa, nauza a kumudzi ndi kumiraga yace.

35 Ndipo iwo anaturuka kukaona cimene cinacitika; ndipo anadza kwa Yesu, nampeza munthuyo, amene ziwanda zinaturuka mwa iye, alikukhala pansi ku mapazi ace a Yesu wobvala ndi wa nzeru zace; ndipo iwo anaopa.

36 Ndipo amene anaona anawauza iwo maciritsidwe ace a wogwidwa ciwandayo.

37 Ndipo anthu aunyinji onse a dziko la Agerasa Ioyandikira anamfunsa iye acoke kwa iwo; cifukwa anagwidwa ndi mantha akuru. Ndipo iye analowa m'ngalawa, nabwerera.

38 Ndipo munthuyo amene ziwanda zinaturuka mwa iye anampempha iye akhale ndi iye; koma anamuuza apite, nanena,

39 Pita kunyumba kwako, nufotokozere zazikuruzo anakucitira iwe Mulungu. Ndipo iye anacoka, nalalikira ku mudzi wonse zazikuruzo Yesu anamcitira iye,

40 Ndipo pakubwera Yesu, khamu la anthu linamlandira iye; pakuti onse analikumlindira iye.

41 Ndipo onani, panadza munthu dzina lace Yairo, ndipo iye ndiye mkuru wa sunagoge; ndipo anagwa pamapazi ace a Yesu, nampempha iye adze kunyumba kwace;

42 cifukwa anali naye mwana wamkazi mmodzi yekha, wa zaka zace ngati khumi ndi ziwiri, ndipo analinkumwalira iye, Koma pakupita iye anthu a mipingo anakanikizana naye,

43 Ndipo mkazi, anali ndi nthenda yacidwalire zaka khumi ndi ziwiri, amene adasudzula asing'anga za moyo wace zonse, ndipo sanathe kuciritsidwa ndi mmodzi yense,

44 anadza pambuyo pace, nakhudza mphonje yacobvala cace; ndipo pomwepo nthenda yace inaleka.

45 Ndipo Yesu anati, Wandikhudza Ine ndani? Koma pamene onse anakana, Petro ndi iwo akukhala naye anati, Ambuye, anthu aunyinji alikukankhana pa Inu ndi kukanikizana.

46 Koma Yesu anati, Wina wandikhudza Ine; pakuti a ndazindikira Ine kuti mphamvu yaturuka mwa Ine.

47 Ndipo mkaziyo pakuona kuti sanabisika, anadza ndi kunthunthumira, nagwa pamaso pace, nafotokoza pamaso pa anthu onsewo cifukwa cace ca kumkhudza iye, ndi kuti anaciritsidwa pomwepo.

48 Ndipo iye anati kwa iyeyu, Mwana wanga, cikhulupiriro cako cakupulumutsa iwe; muka ndi mtendere.

49 M'mene iye anali cilankhulire, anadza wina wocokera kwa mkuru wa sunagoge, nanena, Mwana wako wafa; usambvute Mphunzitsi.

50 Koma Yesu anamva, namyankha, kuti, Usaope; khulupira kokha, ndipo iye adzapulumutsidwa.

51 Ndipo pakufika iye kunyumbako, sanaloleza wina kulowa naye pamodzi, koma Petro, ndi Yohane, ndi Yakobo, ndi atate wa mwanayo, ndi amace.

52 Ndipo anthu onse analikumlira iye ndi kudzigugudapacifuwa. Koma iye anati, Musalire; pakuti iye sanafa, koma agona tulo.

53 Ndipo anamseka iye pwepwete podziwa kuti anafa.

54 Ndipo iye anamgwira dzanja lace, naitana, nati, Buthu, tauka.

55 Ndipo mzimu wace unabwera, ndipo anauka pomwepo; ndipo iye anawauza kuti ampatse kanthu ka kudya.

56 Ndipo atate wace ndi amace anadabwa; ndipo analamulira iwo asauze munthu ali yense cimene cinacitika.

9

1 Ndipo iye anaitana pamodzi khumi ndi awiriwo nawapatsa mphamvu ndi ulamuliro pa ziwanda zonse, ndi zakuciritsa nthenda.

2 Ndipo anawatuma kukalalikira Ufumu wa Mulungu, ndi kuciritsa anthu odwala.

3 Ndipo iye anati kwa iwo, Musanyamule kanthu ka paulendo, kapena ndodo, kapena thumba, kapena mkate, kapena ndarama; ndipo musakhale nao malaya awiri.

4 Ndipo m'nyumba iri yonse mukalowemo, khalani komweko, ndipo muzikacokera kumeneko.

5 Ndipo onse amene sakakulandireni inu, m'mene muturuka m'mudzi womwewo, sansani pfumbi la pa mapazi anu, likhale mboni ya paiwo.

6 Ndipo iwo anaturuka, napita m'midzi m'midzi, ndi kulalikira Uthenga Wabwino, ndi kuciritsa ponse.

7 Ndipo Herode ciwangaco anamva mbiri yace ya zonse zinacitika; ndipo inamthetsa nzeru, cifukwa ananena anthu ena, kuti Yohane anauka kwa akufa;

8 koma ena, kuti Eliya anaoneka; ndipo ena, kuti mneneri wina wa akale aja anauka.

9 Ndipo Herode anati, Yohane ndinamdula mutu ine; koma uyu ndani ndikumva zotere za iye? Ndipo anafunafuna kumuona iye.

10 Ndipo atabwera atumwi, anamfotokozera iye zonse anazicita. Ndipo iye anawatenga, napatuka nao pa okha kunka ku mudzi dzina lace Betsaida.

11 Koma unyinji wa anthu, pamene anadziwa, anamtsata Iye; ndipo iye anawalandira, nalankhula nao za Ufumu wa Mulungu, naciritsa amene anasowa kuciritsidwa.

12 Koma dzuwa lidapendeka; ndipo khumi ndi awiriwo anadza, nati kwa iye, Tauzani makamu a anthu amuke, kuti apite ku midzi yoyandikira ndi kumiraga, kukafuna pogona, ndi kupeza zakudya; cifukwa tiri ku malo acipululu kuno.

13 Koma anati kwa iwo, Muwapatse kudya ndinu. Koma anati, Ife tiribe mikate, koma isanu yokha, ndi nsomba ziwiri zokha; kapena timuke ife kukagulira anthu awa onse zakudya.

14 Pakuti anali amuna ngati zikwi zisanu. Koma iye anati kwa ophunzira ace, Khalitsani iwo pansi magulu magulu, ngati makumi asanu asanu.

15 Ndipo anatero, nawakhalitsa pansi onsewo.

16 Ndipo iye, m'mene anatenga mikate isanu ija ndi nsomba ziwiri anayang'ana kumwamba, nazidalitsa, nanyema, napatsa ophunzira apereke kwa anthuwo.

17 Ndipo anadya, nakhuta onsewo; natola makombo, mitanga khumi ndi iwiri.

18 Ndipo kunali, pamene iye analikupemphera padera, ophunzira anali naye; ndipo anawafunsa iwo, kuti, Makamuwo a anthu anena kuti Ine ndine yani?

19 Ndipo anayankha nati, Yohane Mbatizi; koma ena, Eliya; ndi ena, kuti anauka mmodzi wa aneneri akale.

20 Ndipo anati kwa iwo, Koma inu munena kuti Ine ndine yani? Ndipo anayankha Petro, nati, Kristu wa Mulungu.

21 Ndipo iye anawauzitsa iwo, nalamulira kuti asanene ici kwa munthu ali yense;

22 nati, Kuyenera kuti Mwana wa munthu amve zowawa zambiri, ndi kukanidwa ndi akuru, ndi ansembe akuru, ndi alembi, ndi kuphedwa, ndi kuuka tsiku lacitatu.

23 Ndipo iye ananena kwa onse, Ngati munthu afuna kudza pambuyo panga, adzikanize yekha, nanyamule mtanda wace tsiku ndi tsiku, nanditsate Ine.

24 Pakutiamene ali yense akafuna kupulumutsa moyo wace, iye adzautaya; koma amene ali yense akataya moyo wace cifukwa ca Ine, iye adzaupulumutsa uwu.

25 Pakuti munthu apindulanji, akadzilemezera dziko lonse lapansi nadzitayapo, kapena kulipapo moyo wace?

26 Pakuti amene ali yense: adzacita manyazi cifukwa ca Ine ndi mau anga, Mwana wa munthu adzacita manyazi cifukwa ca iye, pamene adzafika ndi ulemerero wace ndi wa Atate, ndi wa angelo oyera.

27 Koma Ine ndinena ndi inu zoonadi, Kuli ena a iwo akuimirira pano, amene sadzalawatu imfa, kufikira kuti adzaona Ufumu wa Mulungu.

28 Ndipo pamene padatha ngati masiku asanu ndi atatu atanena mau amenewa, Iye anatenga Petro ndi Yohane ndi Yakobo apite naye, nakwera m'phiri kukapemphera.

29 Ndipo m'kupemphera kwace, maonekedwe a nkhope yace anasandulika, ndi cobvala cace cinayera ndi kunyezimira.

30 Ndipo onani, analikulankhulana nayeamuna awiri, ndiwo Mose ndi Eliya;

31 amene anaonekera m'ulemerero, nanenaza kumuka kwace kumene iye ati adzatsiriza ku Yerusalemu.

32 Koma Petro ndi iwo anali naye analemedwa ndi tulo; koma m'mene anayera m'maso ndithu, anaona ulemerero wace, ndi amuna awiriwo akuimirira ndi iye.

33 Ndipo panali polekana iwo aja ndi iye, Petro anati kwa Yesu, Ambuye, nkwabwino kuti tiri pano; ndipo timange misasa itatu, umodzi wa Inu, ndi wina wa Mose, ndi wina wa Eliya; wosadziwa iye cimene alikunena.

34 Ndipo akadalankhula izi, unadza mtambo, nuwaphimba iwo; ndipo anaopa pakulowa iwo mumtambo.

35 Ndipo munaturuka mau mumtambo nanena, Uyu ndiye Mwana wanga, wosankhidwayo; mverani iye.

36 Ndipo pakutero mauwo, Yesu anapezedwa ali yekha. Ndipo iwo anakhala cete, ndipo sanauza munthu ali yense masiku aja kanthu konse ka izo anaziona.

37 Ndipo panali, m'mawa mwace, atatsika m'phiri, khamu lalikuru la anthu linakomana naye.

38 Ndipo onani, anapfuula munthu wa m'khamulo, nanena, nati, Mphunzitsi, ndikupemphani, yang'anirani mwana wanga; cifukwa ndiye mmodzi yekha wa ine:

39 ndipo onani, umamgwira iye mzimu, napfuula modzidzimuka; ndipo umamng'amba iye ndi kumcititsa thobvu pakamwa, nucoka pa iye mwa unyenzi, numgola iye.

40 Ndipo ndinapempha ophunzira anu kuti auturutse; koma sanathe.

41 Ndipo Yesu anayankha, nati, Ha! obadwa inu osakhulupirira ndi amphulupulu, ndidzakhala ndi inu nthawi yanji, ndi kulekerera inu? idza naye kuno mwana wako.

42 Ndipo akadadza iye, ciwandaco cinamgwetsa, ndi kumng'ambitsa, Koma Yesu anadzudzula mzimu wonyansawo, naciritsa mnyamata, nambwezera iye kwa atate wace.

43 Ndipo onse anadabwa pa ukulu wace wa Mulungu. Koma pamene onse analikuzizwa ndi zonse anazicita, iye anati kwa ophunzira ace,

44 Alowe mau ame: newa m'makutu anu; pakuti Mwana wa munthu adzaperekedwa m'manja a anthu.

45 Koma iwo sanadziwitse mau awa, ndipo anabisidwa kwa iwo, kuti asawadziwe; ndipo anaopa kumfunsa za mau awa.

46 Ndipo anayamba kutsutsana kuti wamkulu mwa iwo ndani.

47 Koma Yesu pakuona kutsutsana kwa mitima yao, anatenga kamwana, nakaimika pambali pace, nati kwa iwo,

48 Amene ali yense akalandire kamwana aka m'dzina langa alandira Ine; ndipo amene andilandira Ine alandira iye amene anandituma Ine; pakuti iye wakukhala wamng'onong'ono wa inu nonse, yemweyu ndiye wamkuru.

49 Ndipo Yohane anayankha nati, Ambuye, tinaona wina alikuturutsa ziwanda m'dzina lanu; ndipo tinamletsa, cifukwa satsatana nafe.

50 Koma Yesu anati kwa iye, Musamletse, pakuti iye amene satsutsana nanu athandizana nanu.

51 Ndipo panali, pamene anayamba kukwanira masiku akuti alandiridwe iye kumwamba, Yesu anatsimika kuloza nkhope yace kunka ku Yerusalemu,

52 natumiza amithenga patsogolo pace; ndipo ananka, nalowa m'mudzi wa Asamariya, kukamkonzera iye malo.

53 Ndipo iwo sanamlandira iye, cifukwa nkhope yace inali yoloza kunka ku Yerusalemu.

54 Ndipo pamene ophunzira ace Yakobo ndi Yohane anaona, anati, Ambuye, Kodi mufuna kuti ife tiuze mota utsike kumwamba ndi kuwanyeketsa iwo?

55 Koma iye anapotoloka nawadzudzula.

56 Ndipo anapita kumudzi kwina.

57 Ndipo m'mene iwo analikuyenda m'njira, munthu anati kwa iye, Ine ndidzakutsatani kumene kuli konse mukapitako.

58 Ndipo Yesu anati kwa iye, Nkhandwe ziri nazo nkhwimba, ndi mbalame za kumwamba zisa, koma Mwana wa munthu alibe potsamira mutu.

59 Ndipo anati kwa munthu wina, Unditsate Ine. Koma iye anati, Mundilole ine, Ambuye, ndithange ndamuka kuika maliro a atate wanga.

60 Koma anati kwa iye, Leka akufa aike akufa a eni okha; koma muka iwe nubukitse mbiri yace ya Ufumu wa Mulungu.

61 Ndipo winanso anati, Ambuye ndidzakutsatani Inu; koma muthange mwandilola kulawirana nao a kunyumba kwanga.

62 Koma Yesu anati kwa iye, Palibe munthu wakugwira cikhasu, nayang'ana za kumbuyo, ayenera Ufumu wa Mulungu.

10

1 Zitatha izi Ambuye anaika ena makumi asanu ndi awiri, nawatuma iwo awiri awiri pamaso pace ku mudzi uli wonse, ndi malo ali onse kumene ati afikeko mwini.

2 Ndipo ananena kwa iwo, Dzinthu dzicuruka, koma anchito acepa; potero pemphani Mwini dzinthu, kuti akankhe anchito kukututa kwace.

3 Mukani; taonani, Ine ndituma inu ngati ana a nkhosa pakati pa mimbulu.

4 Musanyamule thumba la ndalama kapena thumba la kamba, kapena nsapato; nimusalankhule munthu panjira.

5 Ndipo m'nyumba iri yonse mukalowamo muthange mwanena, Mtendere ukhale pa nyumba iyi.

6 Ndipo mukakhala mwana wa mtendere m'menemo, mtendere wanu udzapumula pa iye; koma ngati mulibe, udzabwerera kwa inu.

7 Ndipo m'nyumba momwemo khalani, ndi kudya ndi kumwa za kwao; pakuti wanchito ayenera mphotho yace; musacokacoka m'nyumba.

8 Ndipo m'mudzi uli wonse mukalowamo, ndipo alandira inu, idyani zomwezi akupatsani;

9 ndipo ciritsani odwala ali mamwemonimunene nao, Ufumu wa Mulungu wayandikira kwa inu. Koma ku mudzi uli wonse mukalowako,

10 ndipo salandira inu, m'mene mwaturuka ku makwalala ace nenani,

11 Lingakhale pfumbi locokera kumudzi kwanu, lomamatika ku mapaziathu, tilisansira pa inu; koma zindikirani ici, kuti Ufumu wa Mulungu wayandikira.

12 Ndinena ndi inu kuti tsiku lijalo ku Sodoma kudzapiririka kuposa mudzi umenewo.

13 Tsoka iwe, Korazini! tsoka iwe Betsaida! cifukwa kuti zikadacitika m'Turo ndi Sidoni zamphamvuzi zidacitika mwa inu, akadalapa kale lomwe ndi kukhala pansi obvala ciguduli ndi phulusa.

14 Koma ku Turo ndi Sidoni kudzapiririka m'ciweruziro, koposa inu.

15 Ndipo iwe, Kapernao, kodi udzakwezedwa kufikira Kumwamba? Udzatsitsidwa kufikira ku Hade,

16 iye wakumvera inu, andimvera Ine; ndipo iye wakukana inu, andikana Ine; ndipo iye wakukana Ine amkana iye amene anandituma Ine.

17 Ndipo makumi asanu ndi awiri aja anabwera mokondwera, nanena, Ambuye, zingakhale ziwanda zinatigonjera ife m'dzina lanu.

18 Ndipo anati kwa iwo, Ndinaona Satana alinkugwa ngati mphezi wocokera kumwamba.

19 Taonani, ndakupatsani ulamuliro wakuponda pa njoka ndi zinkhanira, ndi pa mphamvu iri yonse ya mdaniyo; ndipo kulibe kanthu kadzakuipsani konse.

20 Koma musakondwera nako kuti mizimu idakugonjerani, koma kondwerani kuti maina anu alembedwa m'Mwamba.

21 Nthawi yomweyo iye anakondwera ndi Mzimu Wovera, nati, Ndikubvomerezani Inu, Atate, Ambuye wa kumwamba ndi wa dziko, kuti izi munazibisira anzeru ndi ozindikira, ndipo munaziululira ana amakanda; indedi, Atate, pakuti kotero kudakondweretsa pamaso panu.

22 Zonse zaperekedwa kwa Ine ndi Atate wanga; ndipo palibe munthu azindikira Mwana ali yani, koma Atate; ndipo Atate ali yani, koma Mwana, ndi iye amene Mwana afuna kumuululira iye.

23 Ndipo m'mene anapotolokera kwa ophunzira ace, ali pa okha, anati, Odala masowo akuona zimene muona.

24 Pakuti ndinena ndi inu kuti 1 aneneri ndi mafumu ambiri anafuna kuona zimene inu muziona, koma sanaziona; ndi kumva zimene mukumva, koma sanazimva.

25 Ndipo taonani, wacilamulo wina anaimirira namuyesa iye, nanena, 2 Mphunzitsi, ndidzalowa moyo wosatha ndi kucita ciani?

26 Ndipo anati kwa iye, M'cilamulo mulembedwa ciani? Uwerenga bwanji?

27 Ndipo iye anayankha nati, 3 Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu yako yonse, ndi nzeru zako zonse, ndi mnansi wako monga iwe mwini.

28 Ndipo anati kwa iye, Wayankha bwino; cita ici, ndipo udzakhala ndi moyo.

29 Koma iye, pofuna kudziyesa yekha wolungama, anati kwa Yesu, Ndipo mnansi wanga ndani?

30 Ndipo Yesu anamlanda mau, nati, Munthu wina anatsika kucokera ku Yerusalemu kunka ku Yeriko; ndipo anagwa m'manja a acifwamba amene anambvula zobvala, namkwapula, nacoka atamsiya wofuna kufa.

31 Ndipo kudangotero kuti wansembe wina anatsika njirayo, ndipo pakumuona iye anapita mbali yina.

32 Momwemonso Mlevi, pofika pamenepo, ndi kumuona, anapita mbali yina.

33 Koma Msamariya wina ali pa ulendo wace anadzapali iye; ndipo pakumuona, anagwidwa cifundo,

34 nadza kwa iye, namanga mabala ace, nathirapo mafuta ndi vinyo; ndipo anamuika iye pa nyama yace ya iye yekha, nadza naye ku nyumba ya alendo, namsungira.

35 Ndipo m'mawa mwace anaturutsa marupiya atheka awiri napatsa mwini nyumba ya alendo, nati, Msungire iye, ndipo ciri conse umpatsa koposa, ine, pobwera, ndidzakubwezera iwe.

36 Uti wa awa atatu, uyesa iwe, anakhala mnansi wa iye uja adagwa m'manja a acifwamba?

37 Ndipo anati, iye wakumcitira cifundo. Ndipo Yesu anati kwa iye, Pita, nucite iwe momwemo.

38 Ndipo pakupita paulendo pao iye analowa m'mudzi wina; ndipo mkazi wina dzina lace 4 Marita anamlandira iye kunyumba kwace.

39 Ndipo anali ndi mbale wace wochedwa Mariya, ndiye wakukhala pa mapazi a Ambuye, namva mau ace.

40 Koma Marita anatekeseka ndi kutumikira kwambiri; ndipo anadzako nati, Ambuye, kodi simusamala kuti mbale wanga anandisiya nditumikire ndekha? Mumuuze tsono kuti andithandize.

41 Koma Ambuye anayankha nati kwa iye, Marita, Marita, uda nkhawa nubvutika ndi zinthu zambiri;

42 koma cisoweka cinthu cimodzi, pakuti Mariya anasankha dera lokoma limene lsilidzacotsedwa kwa iye.

11

1 Ndipo kunali, pakukhala iye pamalo pena ndi kupemphera, m'mene analeka, wina wa ophunzira ace anati kwa iye, Ambuye, tiphunzitseni ife kupemphera, monganso Yohane anaphunzitsa ophunzira ace.

2 Ndipo anati kwa iwo, M'mene mupemphera nenani, Atate, Dzina lanu liyeretsedwe; Ufumu wanu udze;

3 tipatseni ife tsiku ndi tsiku cakudya ca patsiku.

4 Ndipo mutikhululukire ife macimo athu; pakuti ifenso tikhululukira munthu yense wa mangawa athu. Ndipo musatitengere ife kokatiyesa.

5 Ndipo anati kwa iwo, Ndani wa inu adzakhala ndi bwenzi lace, nadzapita kwa iye pakati pa usiku, nadzati kwa iye, Bwenzi, ndibwereke mikate itatu;

6 popeza wandidzera bwenzi langa locokera paulendo, ndipo ndiribe compatsa;

7 ndipo iyeyu wa m'katimo poyankha akati, Usandibvuta; pakhomo mpotseka tsopano, ndipo ana anga ali nane pamodzi pogona; sindikhoza kuuka ndi kukupatsa?

8 Ndinena ndi inu, ngakhale sadzauka ndi kumpatsa, cifukwa ali bwenzi lacevkoma cifukwa ca liuma lace adzauka nadzampatsa iye ziri zonse azisowa.

9 Ndipo Ine ndinena ndi inu, Pemphani, ndipo adzakupatsani; funani, ndipo mudzapeza; gogodani ndipo adzakutsegulirani.

10 Pakuti yense wakupempha alandira; ndi wofunayo apeza; ndi iye amene agogoda adzamtsegulira.

11 Ndipo ndani wa inu ali atate, mwana wace akadzampempha mkate, adzampatsa mwala? kapena nsomba, nadzamninkha njoka m'malo mwa nsomba?

12 kapena akadzampempha dzira kodi adzampatsa cinkhanira?

13 Potero, ngati inu, okhala oipa, mudziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, koposa kotani nanga Atate wanu wa Kumwamba adzapatsa Mzimu Woyera kwa iwo akumpempha iye?

14 Ndipo analikuturutsa ciwanda cosalankhula. Ndipo kunali, citaturuka ciwanda, wosalankhulayo analankhula; ndipo makamu a anthu anazizwa.

15 Koma ena mwa iwo anati, Ndi Beelzebule mkuru wa ziwanda amaturutsa ziwanda.

16 Koma ena anamuyesa, nafuna kwa iye cizindikilo cocokera Kumwamba.

17 Koma iye, podziwa zolingirira zao, anati kwa iwo, Ufumu uli wonse wogawanika m'kati mwace upasuka; ndipo nyumba ikagawanika m'kati mwace igwa.

18 Ndiponso ngati Satana agawanika kudzitsutsa mwini, udzaimika bwanji ufumu wace? popeza munena kuti nditurutsa ziwanda ndi Beelzebule.

19 Koma ngati Ine ndimaturutsa ziwanda ndi Beelzebule, ana anu aziturutsa ndi yani? Mwa ici iwo adzakhala oweruza anu.

20 Koma ngati Ine nditurutsa ziwanda ndi cala ca Mulungu, pamenepo Ufumu wa Mulungu wafikira inu.

21 Pamene pali ponse mwini mphamvu alonda pabwalo pace zinthu zace ziri mumtendere;

22 koma pamene pali ponse amdzera wakumposa mphamvu, nakamlaka, amcotsera zida zace zonse zimene anazitama, nagawa zofunkha zace.

23 Iye wosabvomerezana ndi Ine atsutsana ndi Ine; ndipo iye wosasonkhanitsa pamodzi ndi Ine amwaza.

24 Pamene pali ponse mzimu wonyansa ukaturuka mwa munthu, upyola malo opanda madzi nufunafuna mpumulo; ndipo posaupeza unena, Ndidzabwera kunyumba kwanga kumene ndinaturukako;

25 ndipo pofika, uipeza yosesa ndi yokonzeka.

26 Pomwepo, upita nutenga mizimu yina isanu ndi iwiri yoipa yoposa ndi uwu mwini; ndipo ilowa nikhalira komweko; ndipo makhalidwe otsiriza a munthu uyu aipa koposa oyambawo.

27 Ndipo kunali, pakunena izi iye, mkazi wina mwa khamu la anthu anakweza mau, nati kwa iye, Yodala mimba imene idakubalani, ndi mawere amene munayamwa.

28 Koma iye anati, Inde, koma odala iwo akumva mau a Mulungu, nawasunga.

29 Ndipo pakusonkhana pamodzi makamu a anthu, anayamba kunena, Mbadwo uno ndi mbadwo woipa; ufuna cizindikilo, ndipo cizindikilo sicidzapatsidwa kwa uwu koma cizindikilo ca Yona.

30 Pakuti monga ngati Yona anali cizindikilo kwa Anineve, cotero adzakhalanso Mwana wa munthu kwa mbadwo uno.

31 Mfumu yaikazi ya kumwera idzaimirira pa mlandu wotsiriza pamodzi ndi amuna a mbadwo uno, nadzawatsutsa; pakuti anadza ku'cokera ku malekezero a dziko kudzamva nzeru za Solomo; ndipo onani, woposa Solomo ali pano.

32 Amuna a ku Nineve adzaimirira pa mlandu wotsiriza pamodzi ndi anthu a mbadwo uno, nadzawatsutsa; pakuti iwo analapa pa kulalikira kwa Y ona; ndipo onani, wakuposa Y ona ali pano.

33 Palibe munthu, atayatsa nyali, aiika m'cipinda capansi, kapena pansi pa muyeso, koma pa coikapo cace, kuti iwo akulowamo aone kuunika.

34 Nyali ya thupi ndiyo diso lako; pamene pali ponse diso lako liri langwiro thupi lako lonse liunikidwanso monsemo; koma likakhala loipa, thupi lako lomwe liri la mdima wokha wokha.

35 Potero yang'anira kuunika kuli mwa iwe kungakhale mdima.

36 Pamenepo, ngati thupi lako lonse liunikidwa losakhala nalo dera lace lamdima, lidzakhala lounikidwa monsemo, ngati pamene nyali ndi kuwala kwace ikuunikira iwe.

37 Ndipo pakulankhula iye, anamuitana Mfarisi kuti adye naye; ndipo analowa naseama kudya.

38 Ndipo anazizwa Mfarisiyo, pakuona kuti anayamba cakudya asanasambe.

39 Koma Ambuye anati kwa iye, Tsopano inu Afarisi muyeretsa kunja kwace kwa cikho ndi mbale, koma m'kati mwanu mudzala zolanda ndi zoipa.

40 Opusa inu, kodi iye wopanga kunja kwace sanapanganso m'kati mwace?

41 koma patsani mphatso yacifundo za m'katimo; ndipo onani, zonse ziri zoyera kwa inu.

42 Koma tsoka inu, Afarisi! cifukwa mupereka limodzi la magawo khumi la timbeu tonunkhira, ndi timbeu tokometsa cakudya ndi ndiwo zonse, ndipo mumaleka ciweruziro ndi cikondi ca Mulungu; mwenzi mutacita izi, ndi kusasiya zinazo.

43 Tsoka inu, Afarisi! cifukwa mukonda mipando yaulemu m'masunagoge, ndi kulankhulidwa m'misika.

44 Tsoka inu! cifukwa muli ngati manda osaoneka, ndipo anthu akuyendayenda pamwamba pao sadziwa,

45 Ndipo mmodzi wa acilamulo anayankha, nanena kwa iye, Mphunzitsi, ndi kunena izi, mutitonza ifenso.

46 Ndipo anati, Tsoka inunso, acilamulo inul cifukwa musenzetsa anthu akatundu osautsa ponyamula, ndipo inu nomwe simukhudza akatunduwo ndi cala canu cimodzi.

47 Tsoka inu! cifukwamumanga za pa manda a aneneri, ndipo makolo anu anawapha.

48 Comweco muli mboni, ndipo mubvomera nchito za makolo anu; cifukwa iwotu anawapha, koma inu muwamangira iwo zapamanda.

49 Mwa icinso nzeru ya Mulungu inati, Ndidzatumiza kwa iwo aneneri ndi atumwi; ndipo ena a iwo adzawapha, nadzawazunza;

50 kuti mwazi wa aneneri onse, wakhetsedwa kuyambira kukhazika kwa dziko lapansi, ukafunidwe kwa anthu a mbadwo uno;

51 kuyambira mwazi wa 1 Abele kufikira mwazi wa 2 Zakariya, amene anamphera pakati pa guwa la nsembe ndi nyumba ya Kacisi. Indetu, ndinena kwa inu udzafunidwa kwa anthu a mbadwo uno.

52 3 Tsoka inu, acilamulo! cifukwa munacotsa cifungulo ca nzeru; inu simunalowamo nokha, ndipo munawaletsa iwo analinkulowa.

53 Ndipo pamene iye anaturuka m'menemo, alembi ndi Afarisi anayamba kumuumiriza iye kolimba, ndi kumtompha iye ndi zinthu zambiri;

54 4 namlindira akakole kanthu koturuka m'kamwa mwace.

12

1 Pomwepo pamene anthu a zikwi zikwi a khamu anasonkhana pamodzi, kotero kuti anapondana, iye anayamba kunena kwa ophunzira ace poyamba, Tacenierani nokha ndi cotupitsa mikate ca Afarisi, cimeneciri cinyengo.

2 Koma kulibe kanthu kobvundikiridwa kamene sikadzaululidwa; ndi kobisika kamene sikadzadziwika.

3 Cifukwa cace zonse zimene mwazinena mumdima zidzamveka poyera; ndipo cimene mwalankhula m'khutu, m'zipinda za m'kati cidzalalikidwa pa macindwi a nyumba.

4 Ndipo ndinena kwa inu, abwenzi anga, Musaope iwo akupha thupi, ndipo akatha ici alibe kanthu kena angathe kucita.

5 Koma ndidzakulangizani amene muzimuopa; taopani iye amene atatha kupha ali ndi mphamvu yakutaya kugehena, inde, ndinena ndinu opani ameneyo.

6 Kodi mpheta zisanu sizigulidwa timakobiri tiwiri? ndipo palibe imodzi ya izo iiwalika pamaso pa Mulungu;

7 komatu ngakhale matsitsi onse a pamutu panu awerengedwa. Musaopa, muposa mtengo wace wa mpheta zambiri.

8 Ndipo ndinena kwa inu, Amene ali yense akabvomereza Ine pamaso pa anthu, inde, Mwana wa munthu adzambvomereza iye pamaso pa angelo a Mulungu;

9 koma iye wondikana Ine pamaso pa anthu, iye adzakanidwa pamaso pa angelo a Mulungu.

10 Ndipo amene ali yense adzanenera Mwana wa munthu zoipa adzakhululukidwa; koma amene anenera Mzimu Woyera zamwano sadzakhululukidwa.

11 Ndipo pamene pali ponse adzamuka nanu ku mlandu wa m'sunagoge ndi kwa akulu, ndi aulamuliro, musade nkhawa ndi kuti mukadzikanira bwanji, ndipo ndi mau otani, kapena mukanena ciani;

12 pakuti Mzimu Woyera adzaphunzitsa inu nthawi yomweyo zimene muyenera kuzinena.

13 Ndipo munthu wa m'khamulo anati kwa iye, Mphunzitsi, uzani mbale wanga agawane ndi ine cuma camasiye.

14 Koma anati kwa iye, Munthu iwe, ndani anandiika Ine ndikhale woweruza, kapena wakugawira inu?

15 Ndipo iye anati kwa iwo, Yang'anirani, mudzisungire kupewa msiriro uli wonse; cifukwa moyo wace wa munthu sulingana ndi kucuruka kwa zinthu zace ali nazo.

16 Ndipo iye ananena nao fanizo, kuti, Munda wace wa munthu mwini cuma unapatsa bwino.

17 Ndipo anaganizaganiza mwa yekha nanena, Ndidzatani ine, popeza ndiribe mosungiramo zipatso zanga?

18 Ndipo anati, Ndidzatere: ndidzapasula nkhokwe zanga, ndi kumanganso zazikuru, ndipo ndidzasungiramo dzinthu zanga zonse, ndi cuma canga.

19 Ndipo ndidzati kwa moyo wanga, Moyo iwe, uli naco cuma cambiri cosungika kufikira zaka zambiri; tapumulatu, nudye, numwe, nukondwere.

20 Koma Mulungu anati kwa iye, Wopusa iwe, usiku womwe uno udzafunidwa moyo wako; ndipo zinthu zimene unazikonza zidzakhala za yani?

21 Atero iye wakudziunjikira cuma mwini yekha wosakhala naco cuma ca kwa Mulungu,

22 Ndipo Iyeanati kwa ophunzira ace, Cifukwa cace ndinena ndinu, Musade nkhawa ndi moyo wanu, cimene mudzadya; kapena ndi thupi lanu, cimene mudzabvala.

23 Pakuti moyo uli woposa cakudya, ndi thupi liposa cobvala.

24 Lingirirani makungubwi, kuti samafesai, kapena kutemai; alibe nyumba yosungiramo, kapena nkhokwe; ndipo Mulungu awadyetsa: nanga inu simuziposa mbalame kwambiri!

25 Ndipo ndani wa inu, ndi kuda nkhawa angathe kuonjeza mkono pa msinkhu wace?

26 Kotero ngati simungathe ngakhale cacing'onong'ono, muderanji nkhawa cifukwa ca zina zija?

27 Lingalirani maluwa, makulidwe ao; sagwiritsa nchito ndi kusapota; koma ndinena kwa inu, Ngakhale Solomo, mu ulemerero wace wonse, sanabvala ngati limodzi la awa.

28 Koma ngati Mulungu abveka kotere maudzu a kuthengo akukhala lero, ndipo mawa aponyedwa pamoto; nanga inu sadzakuninkhani koposa, inu okhulupirira pang'ono?

29 Ndipo inu musafunefune cimene mudzadya, ndi cimene mudzamwa; ndipo musakayike mtima.

30 Pakuti izi zonse mitundu ya anthu a pa dziko lapansi amazifunafuna; koma Atate wanu adziwa kuti musowa zimenezi.

31 Komatu tafuna-funani Ufumu wace, ndipo izi adzakuonjezerani.

32 Musaopa, kagulu ka nkhosa inu; cifukwa Atate wanu akonda kukupatsani Ufumu.

33 Gulitsani zinthu muli nazo, nimupatse mphatso zacifundo; mudzikonzere matumba a ndarama amene sakutha, cuma cosatha m'Mwamba, kumene mbala siziyandikira, ndipo njenjete siziononga.

34 Pakuti kumene kuli cuma canu, komweko kudzakhalanso mtima wanu.

35 Khalani odzimangira m'cuuno, ndipo nyali zanu zikhale zoyaka;

36 ndipo inu nokha khalani ofanana ndi anthu oyembekezera mbuye wao, pamene ati abwera kucokera kuukwati; kuti pakudza iye, nakagogoda, akamtsegulire pomwepo.

37 Odala akapolowo amene mbuye wao, pakudza iye, adzawapeza odikira; indetu ndinena ndinu, kuti iye adzadzimangira m'cuuno, nadzawakhalitsa pansi kudya, nadzafika, nadzawatumikira.

38 Ndipo akadza ulonda waciwiri, kapena wacitatu, nakawapeza atero, odala amenewa.

39 Koma zindikirani ici, kuti mwini nyumba akadadziwa nthawi yace yakudza mbala, akadadikira, ndipo sakadalola nyumba yace ibooledwe.

40 Khalani okonzeka inunso; cifukwa nthawi imene simulingirira, Mwana wa munthu akudza.

41 Ndipo Petro anati, Ambuye, kodi fanizo ili mwalinena kwa ife, kapena kwa onse?

42 Ndipo Ambuye anati, Ndani tsono ali mdindo wokhulupirika ndi wanzeru, amene mbuye wace adzamuika kapitao wa pa banja lace, kuwapatsa iwo phoso lao pa nthawi yace?

43 Wodala kapoloyo amene mbuye wace pakufika, adzampeza alikucita cotero.

44 1 Ndinena ndinu zoona, kuti adzamuika iye kapitao wa pa zonse ali nazo.

45 Koma 2 kapolo uyo akanena mumtima mwace, Mbuye wanga azengereza kudza; ndimo akayamba kupanda anyamata ndi adzakazi ndi kudya ndi kumwa, ndi kuledzera;

46 3 mbuye wa kapolouyo adzafika tsiku lakuti samuyembekezera, ndi nthawi yakuti saidziwa, nadzamdula iye pakati, nadzamuika dera lace pamodzi ndi anthu osakhulupirira.

47 Ndipo 4 kapolo uyo, wodziwa cifuniro ca mbuye wace, ndipo sanakonza, ndi kusacita zonga za cifuniro caceco, adzakwapulidwa mikwapulo yambiri.

48 Koma 5 iye amene sanacidziwa, ndipo anazicita zoyenera mikwapulo, adzakwapulidwa pang'ono. Ndipo kwa munthu ali yense adampatsa zambiri, kwa iye adzafuna zambiri; ndipo amene anamuikizira zambiri, adzamuuza abwezere zoposa.

49 Ine ndinadzera kuponya mota pa dziko lapansi; ndipo ndifunanji, ngati unatha kuyatsidwa?

50 Koma ndiri ndi ubatizo ndikabatizidwe nao; ndipo ndikanikizidwa Ine kufikira ukatsirizidwa!

51 Kodi muyesa kuti ndinadzera kudzapatsa mtendere pa dziko lapani? Ndinena wa inu, Iaitu, komatu kutsutsana;

52 pakuti 6 kuyambira tsopano adzakhala m'nyumba imodzi anthu asanu, atatu adzatsutsana ndi awiri, ndi awiri adzatsutsana ndi atatu.

53 Adzatsutsana atate ndi mwana wace, ndi mwana ndi atate wace; amace adzatsutsana ndi mwana wamkazi'l ndi mwana wamkazi ndi amace, mpongozi adzatsutsana ndi mkazi wa mwana wace, ndi mkaziyo ndi mpongozi wace.

54 Koma iye ananenanso kwa makamu a anthu, 7 Pamene pali ponse muona mtambo wokwera kumadzulo, pomwepo munena, kuti, Ikudza mvula; ndipo itero.

55 Ndipo pamene mphepo ya kumwela iomba, munena, kuti, Kudzakhala kutenthatu; ndipo kuterodi.

56 Onyenga inu, mudziwa kuzindikira nkhope yace ya dziko lapansi ndi ya thambo; koma simudziwa bwanji kuzindikira nyengoyino?

57 Ndipo inunso, pa nokha mulekeranji kuweruza kolungama?

58 Pakuti 8 pamene ulikupita naye mnzako wa miandu kwa woweruza, fulumira panjira kutha naye mlandu, kuti angakokere iwe kwa woweruza, ndipo woweruzayo angapereke iwe kwa msilikari, ndi msilikari angaponye iwe m'nyumba yandende.

59 Ine ndinena kwa iwe, 9 Sudzaturukamo konse kufikira utalipira kakobiri kakumariza.

13

1 Ndipo anakhalako nthawi yomweyo, anthu ena amene anamuuza iye za Agalileya, amene Pilato anasanganiza mwazi wao ndi nsembe zao.

2 Ndipo iye anayankha nati kwa iwo, Kodi muyesa kuti Agalileya aja anali anthu akucimwa koposa Agalileya onse, cifukwa anamva zowawa izi?

3 Ndinena kwa inu, iaitu; koma ngati inu simutembenuka mtima, mudzaonongeka nonse momwemo.

4 Kapena iwo aja khumi ndi asanu ndi atatu, amene nsanja yaitali ya m'Siloamu inawagwera, ndi kuwapha; kodi muyesa kuti iwo anali olakwa koposa anthu onse akukhala m'Yerusalemu?

5 Ndinena kwa inu, Iaitu; koma ngati simutembenuka mtima, mudzaonongeka nonse ci, modzimodzi.

6 Ndipo iye ananena fanizo ili: Munthu wina anali ndi mkuyu wookam'munda wace wamphesa. Ndipo anadza nafuna cipatso pa uwu, koma anapeza palibe.

7 Ndipo anati kwa wosungira munda wamphesa, Taona, zaka zapita zitatu ndimadza ine kudzafuna cipatso pa mkuyu uwu, ndipo ndimapeza palibe: taulikha; uyeseranjinso nthaka yopanda pace?

8 Ndipo iye anayankha nanena naye, Mbuye, baulekani ngakhale caka cino comwe, kufikira ndidzaukumbira kwete, ndithirepo ndowe;

9 ndipo, ngati udzabala cipatso kuyambira pamenepo, cabwino; koma ngati iai, mudzaulikhatu.

10 Ndipo analikuphunzitsa m'sungagoge mwina, tsiku la Sabata.

11 Ndipo mkazi anali nao mzimu wakumdwalitsa zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu; nakhala wopeteka, ndimo analibe mphamvu konse yakuweramuka.

12 Ndipo Yesu m'mene anamuona, anamuitana, nanena naye, Mkaziwe, wamasulidwa kudwala kwako.

13 Ndipo anaika manja ace pa iye; ndipo pomwepo anaongoledwa, nalemekeza Mulungu.

14 Ndipo mkuru wa sunagoge anabvutika mtima, cifukwa Yesu anaciritsa tsiku la Sabata, nayankha, nanena kwa khamulo, Alipo masiku asanu ndi limodzi, m'menemo anthu ayenera kugwira nchito, cifukwa cace idzani kudzaciritsldwa momwemo, koma tsiku la Sabata ai.

15 Koma Ambuye anamyankha iye, nati, Onyenga inu, kodi munthu ali yense wa inu samaimasula ng'ombe yace, kapena buru wace kucodyeramo, tsiku la Sabata, kupita nayo kukaimwetsa madzi?

16 Ndipo mkazi uyu, ndiye mwana wa Abrahamu, amene Satana anammanga, onani, zaka khumi ndi zisanu ndi zitatu, nanga si kuyenera kodi, kuti amasulidwe nsinga yace imeneyi tsiku la Sabata?

17 Ndipo pamene Iye anatero, onse aja akutsutsana naye ananyazitsidwa; ndipo anthu onse a m'khamu anakondwera ndi zinthu zonse za ulemererozo zinacitidwa ndi iye.

18 Pamenepo ananena, Ufumu wa Mulungu ufanana ndi ciani? ndipo ndidzaufanizira ndi ciani?

19 Ufanana ndi kambeu kampiru, kamene munthu anatenga, nakaponya m'munda wace wace, ndipo kanamera, kanakula mtengo; ndi mbalame za m'mlengalenga zinabindikira mu nthambi zace.

20 Ndiponso anati, Ndidzafanizira Ufumu wa Mulungu ndi ciani?

21 Ufanana ndi cotupitsa mikate, cimene mkazianatenga, nacibisa mu miyeso itatu ya ufa, kufikira unatupa wonsewo,

22 Ndipo Iye anapita pakati pa mizinda ndi midzi, naphunzitsa, nayenda ulendo kunkabe ku Yerusalemu.

23 Ndipo munthu anati kwa iye, Ambuye, akupulumutsidwandiwo owerengeka kodi? Koma iye anati kwa iwo,

24 Yesetsani kulowa pa khomo lopapatiza; cifukwa anthu ambiri, ndikuuzani, adzafunafuna kulowamo, koma sadzakhoza.

25 Pamene atauka mwini nyumba natseka pakhomo, ndipo inu mudzayamba kuima pabwalo, ndi kugogoda pacitseko, ndi kunena, Ambuye titsegulireni ife; ndipo iye adzayankha nadzati ndi inu, Sindidziwa inu kumene mucokerako;

26 pomwepo mudzayambakunena, Ifetinadya ndi kumwa pamaso panu, ndipo munaphunzitsa m'makwalala a kwathu;

27 ndipo iye adzati, Ndinena kwa inu, sindidziwa kumene mucokera inu; cokani pa Ine, nonse akucita cosalungama,

28 Kudzakhala komweko kulira ndi kukukuta mano, pamene mudzaona Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo, ndi aneneri onse, mu. Ufumu wa Mulungu, koma inu nokha muturutsidwa kunja.

29 Ndipo anthu adzacokera kum'mawa, ndi kumadzulo, ndi kumpoto, ndi kumwela, nadzakhalapansi mu Ufumu wa Mulungu.

30 Ndipo onani, alipo akuthungo amene adzakhala oyamba, ndipo alipo oyamba adzakhala akuthungo.

31 Nthawi yomweyo anadzapo Afarisi ena, nanena kwa iye, Turukani, cokani kuno; cifukwa Herode afuna kupha lou.

32 Ndipo iye anati kwa iwo, Pitani kauzeni nkhandweyo, Taonani, nditurutsa ziwanda, nditsiriza maciritso lero ndi mawa, ndipo mkuca nditsirizidwa.

33 Komatu ndiyenera ndipite ulendo wanga lero ndi mawa ndi mkuca, cifukwa sikuloleka kuti mneneri aonongeke kunja kwace kwa Yerusalemu.

34 Yerusalemu, Yerusalemu, iwe wakupha aneneri, ndi wakuponya miyala iwo atumidwa kwa iwe! ha! kawiri kawiri ndinafuna kusonkhanitsa ana ako, monga ngati thadzi ndi anapiye ace m'mapiko ace, ndipo simunafunai!

35 onani nyumba yanu isiyidwa kwa inu yabwinja; ndipo ndinena kwa inu kuti, Simudzandiona Ine, kufikira mudzati, Wolemekezeka iye amene akudza m'dzina la Ambuye.

14

1 Ndipo panali pamene iye analowa m'nyumba ya mmodzi wa akuru a Afarisi tsiku la Sabat a, kukadya, iwo analikumzonda iye.

2 Ndipo onani, panali pamaso pace munthu wambulu.

3 Ndipo Yesu anayankha nati kwa acilamulo ndi Afarisi, nanena, Kodi nkuloledwa tsiku la Sabata kuciritsa, kapena iai?

4 Koma iwo anakhala cete. Ndipo anamtenga namciritsa, namuuza apite.

5 Ndipo anati kwa iwo, Ndani wa inu buru wace kapena ng'ombe yace itagwa m'citsime, ndipo sadzaiturutsa pomwepo tsiku la Sabata kodi?

6 Ndipo iwo sanathe kumbwezera mau pa zinthu izi.

7 Ndipo iye ananena fanizo kwa oitanidwa, popenya kuti amadzisankhira mipando yaulemu, nanena kwa iwo,

8 Pamene pali ponse waitanidwa iwe ndi munthu ku cakudya ca ukwati, usaseama pa mpando waulemu; kuti kapena wina waulemu wakuposa iwe akaitanidwe ndi iye,

9 ndipo pakufika iye amene adaitana iwe ndi uyu, adzati kwa iwe, Mpatse uyu malo; ndipo pomwepo udzayamba manyazi kukhala pa mpando wa kuthungo.

10 Koma pamene pali ponse waitanidwa iwe, pita nukhale pansi pa malo a kuthungo; kotero kuti pamene akadza iye anakuitana iwe, akanena ndi iwe, Bwenzi langa, sendera, kwera kuno; pomwepo udzakhala ndi ulemerero pamaso pa onse akuseama pacakudya pamodzi ndi iwe.

11 Cifukwa munthu ali yense wakudzikuza adzacepetsedwa; ndipo wakudzicepetsa adzakulitsidwa.

12 Ndipo ananenanso kwa iye amene adamuitana, Pamene ukonza cakudya ca pausana kapena ca madzulo, usaitane abwenzi ako, kapena abale ako, kapena a pfuko lako, kapena anansi ako eni cuma; kuti kapena iwonso angabwereze kuitana iwe, ndipo udzakhala nayo mphotho.

13 Koma pamene ukonza phwando uitane aumphawi, opunduka, otsimphina, akhungu;

14 ndipo udzakhala wodala; cifukwa iwo alibe cakubwezera iwe mphotho; pakuti idzabwezedwa mphotho pa kuuka kwa oiungama.

15 Ndipo pamene wina wa iwo akuseama pacakudya pamodzi ndi iye anamva izi, anati kwa iye, Wodala iye amene adzadya mkate mu Ufumu wa Mulungu.

16 Koma anati kwa iye, Munthu wina anakonza phwando lalikuru; naitana anthu ambiri;

17 ndipo anatumiza kapolo wace pa nthawi ya phwando kukanena kwa oitanidwawo, idzani, cifukwa zonse zakonzeka tsopano.

18 Ndipo onse ndi mtima umodzi anayamba kuwiringula. Woyamba anati kwa iye, Ine ndagula munda, ndipo ndiyenera ndituruke kukauona; ndikupempha undilole ine ndisafika.

19 Ndipo anati wina, Ine ndagula ng'ombe za magori asanu, ndipo ndinka kukaziyesa; ndikupempha undilole ine ndisafika.

20 Ndipo anati wina, Ine ndakwatira mkazi, ndipo cifukwa cace sindingathe kudza.

21 Ndipo kapoloyo pakubwera anauza mbuye wace zinthu izi. Pamenepo mwini nyumba anakwiya, nati kwa kapolo wace, Turuka msanga, pita kumakwalala ndi ku njira za mudzi, nubwere nao muno aumphawi ndi opunduka ndi akhungu ndi otsimphina.

22 Ndipo kapoloyo anati, Ambuye, cimene munacilamulira cacitika, ndipo malo atsalapo.

23 Ndipo mbuye ananena kwa kapoloyo, Turuka, nupite kumiseu ndi njira za kuminda, nuwaumirize anthu alowe, kuti nyumba yanga idzale.

24 Pakuti ndinena kwa inu, kuti kulibe mmodzi wa amuna oitanidwa aja adzalawa phwando langa.

25 Ndipo mipingo yambiri ya anthu inamuka naye; ndipo iye anapotoloka, nati kwa iwo.

26 Munthu akadza kwa Ine, wosada atate wace ndi amace, ndi mkazi wace, ndi ana, ndi abale, ndi alongo ace, inde ndi moyo wace womwe wa iye mwini, sakhoza kukhala wophunzira wanga.

27 Ndipo amene ali yense sasenza mtanda wace wa mwini yekha, ndi kudza pambuyo panga, sakhoza kukhala wophunzira wanga,

28 Pakuti ndani wa inu amene akafuna kumanga nsanja yaitali, sathanga wakhala pansi, nawerengera mtengo wace, aone ngati ali nazo zakuimariza?

29 Kuti kungacitike, pamene atakhazika pansi miyala ya ku maziko ace, osakhoza kuimariza, anthu onse akuyang'ana adzayamba kumseka iye,

30 ndi kunena kuti, Munthu uyu anayamba kumanga, koma sanathe kumariza.

31 Kapena mfumu yanji pakupita kukomana ndi nkhondo ya mfumu inzace, sathanga wakhala pansi, nafunsana ndi akuru ngati akhoza ndi asilikari ace zikwi khumi kulimbana naye wina uja alikudza kukomana naye ndi asilikari zikwi makumi awiri?

32 Koma ngati sakhoza, atumiza akazembe, pokhala winayo ali kutalitali, nafunsa za mtendere.

33 Cifukwa cace tsono, yense wa inu amene sakaniza zonse ali nazo, sakhoza kukhala wophunzira wanga.

34 Kotero mcere uli wokoma; koma ngati mcere utasukuluka adzaukoleretsa ndi ciani?

35 Suyenera kuuthira pamunda kapena padzala, autaya kunja. Amene ali nao makutu akumva amve.

15

1 Koma amisonkho onse ndi anthu ocimwa analikumyandikira kudzamva iye.

2 Ndipo Afarisi ndi alembi anadandaula nati, Uyu alandira anthu ocimwa, nadya nao.

3 Koma anati kwa iwo fanizo ili, nanena,

4 Munthu ndani wa inu ali nazo nkhosa makumikhumi, ndipo pakutayika imodzi ya izo, sasiya nanga m'cipululu zinazo makumi asanu ndi anai mphambu zisanu ndi zinai, nalondola yotayikayo kufikira aipeza?

5 Ndipo pamene adaipeza, aisenza pa mapewa ace wokondwera.

6 Ndipo pakufika kunyumba kwace amema abwenzi ace ndi anansi ace, nanena nao, Kondwerani ndi ine, cifukwa ndinapeza nkhosa yanga yotayikayo.

7 Ndinena kwa inu, kotero kudzakhala cimwemwe Kumwamba cifukwa ca wocimwa mmodzi wotembenuka mtima, koposa anthu olungama makumi asanu ndi anai mphambu asanu ndi anai, amene alibe kusowa kutembenuka mtima.

8 Kapena mkazi wanji ali nazo ndalama zasiliva khumi, ngati itayika imodzi, sayatsa nyali, nasesa m'nyumba yace, nafunafuna cisamalire kufikira akaipeza?

9 Ndipo m'mene aipeza amema abwenzi ace ndi anansi ace, nanena; Kondwerani ndi ine, cifukwa ndinapeza ndalama ndidatayayo.

10 Comweco, ndinena kwa inu, kuli cimwemwe pamaso pa angelo a Mulungu cifukwa ca munthu wocimwa mmodzi amene atembenuka mtima.

11 Ndipo iye anati, Munthu wina anali ndi ana amuna awiri;

12 ndipo wamng'onoyo anati kwa atate wace, Atate, ndigawirenitu zanga za pa cuma canu. Ndipo iye anawagawira za moyo wace.

13 Ndipo pakupita masiku owerengekamwana wamng'onoyo anasonkhanitsa zonse, napita ulendo wace ku dziko lakutari; ndipo komweko anamwaza cuma cace ndi makhalidwe a citayiko.

14 Ndipo pamene anatha zace zonse, panakhala njala yaikuru m'dziko muja, ndipo iye anayamba kusowa.

15 Ndipo anamuka nadziphatikiza kwa mfulu imodzi ya dziko lija; ndipo uyu anamtumiza kubusa kwace kukaweta nkhumba.

16 Ndipo analakalaka kukhutitsa mimba yace ndi makoko amene nkhumba rimadya, ndipo palibe munthu anamninkha kanthu.

17 Koma m'mene anakumbukila mumtima, anati, Anchito olipidwa ambiri a atate wanga ali naco cakudya cocuruka, ndipo ine ndionongeke kuno ndi njala?

18 Ndidzanyamuka ndipite kwa atate wanga, ndipo ndidzanena nave, Atate, ndinacimwira Kumwamba ndi pamaso panu;

19 sindiyeneranso konse kuchulidwa mwana wanu; mundiyese ine ngati mmodzi wa anchito anu.

20 Ndipo iye ananyamuka, nadza kwa atate wace. Koma pakudza iye kutali, atate wace anamuona, nagwidwa cifundo, nathamanga, namkupatira pakhosi pace, nampsompsonetsa.

21 Ndipo mwanayo anati kwa iye, Atate ndinacimwira Kumwamba ndi pamaso panu, sindiyeneranso konse kuchulidwa mwana wanu.

22 Koma atateyo ananena kwaakapolo ace, Turutsani msanga mwinjiro wokometsetsa, nimumbveke; ndipo mpatseni phete ku dzanja lace ndi nsapato ku apazi ace;

23 ndipo idzani naye mwana wa ng'ombe wonenepa, mumuphe, ndipo tidye, tisekere;

24 cifukwa mwana wanga uyu anali wakufa, ndipo akhalanso wamoyo; anali wotayika, ndipo wapezedwa. Ndipo anayamba kusekera.

25 Koma mwana wace wamkuru anali kumunda. Ndipo pakubwera iye ndi kuyandikira kunyumba, anamva kuyimba ndi kubvina.

26 Ndipo anaitana mmodzi wa anayamata, namfunsa, Zinthu izi nzotani?

27 Ndipo uyu anati kwa iye, Mng'ono wako wafika; ndipo atate wako anapha mwana wa ng'ombe wonenepa, cifukwa anamlandira iye wamoyo.

28 Koma anakwiya, ndipo sanafuna kulowamo, Ndipo atate wace anaturuka namdandaulira.

29 Koma anayankha nati kwa atate wace, Onani, ine ndinakhala kapolo wanu zaka zambiri zotere, ndipo sindinalakwira lamulo lanu nthawi iri yonse; ndipo simunandipatsa ine kamodzi konse mwana wa mbuzi, kuti ndisekere ndi abwenzi anga.

30 Koma pamene anadza mwana wanu uyu, wakutha zamoyo zanu ndi akazi aciwerewere, munamphera iye mwana wa ng'ombe wonenepa.

31 Koma iye ananena nave, Mwana wanga, iwe uli ndine nthawi zonse, ndipo zanga zonse ziri zako.

32 Koma kudayenera kuti tisangalale ndi kukondwerera: cifukwa mng'ono wako uyu anali wakufa ndipo ali ndi moyo; anatayika, ndipo wapezeka.

16

1 Ndipo iye ananenanso kwa ophunzira ace, Panali munthu mwini cuma, anali ndi kapitao wace; ndipo ameneyu ananenezedwa kwa iye kuti alikumwaza cuma cace.

2 Ndipo anamuitana, nati kwa iye, ici ndi ciani ndikumva za iwe? Undiwerengere za ukapitao wako; pakuti sungathe kukhalabe kapitao.

3 Ndipo kapitao uyu anati mumtima mwace, Ndidzacita ciani, cifukwa mbuye wanga andicotsera ukapitao? kulima ndiribe mphamvu, kupemphapempha kundicititsa manyazi.

4 Ndidziwa cimene ndidzacita, kotero kuti pamene ananditurutsa muukapitao, anthu akandilandire kunyumba kwao.

5 Ndipo anadziitanira mmodzi ndi mmodzi amangawa onse a mbuye wace, nanena kwa woyamba, Unakongola ciani kwa mbuye wanga?

6 Ndipo anati, Mitsuko ya mafuta zana. Ndipo iye ananena naye, Tenga kalata wako, nukhale pansi msanga, nulembere, Makumi asanu.

7 Pomwepo anati kwa wina, Ndipo iwe uli nao mangawa otani? Ndipo uyu anati, Mitanga ya tirigu zana iye ananena naye, Tenga kalata wako nulembere makumi asanu ndi atatu.

8 Ndipo mbuye wace anatama kapitao wonyengayo, kuti anacita mwanzeru; cifukwa ana a nthawi ya pansi pano ali anzeru m'mbadwo wao koposa ana a kuunika.

9 Ndipo Ine ndinena kwa inu, Mudziyesere nokha abwenzi ndi cuma cosalungama; kuti pamene cikakusowani, iwo akalandire inu m'mahema osatha.

10 Iye amene akhulupirika m'cacing'onong'ono alinso wokhulupirika m'cacikuru; ndipo iye amene ali wosalungama m'cacing'onong'ono alinso wosalungama m'cacikuru.

11 Cifukwa cace ngati simunakhala okhulupirika m'cuma ca cosalungama, adzakhulupirira inu ndani ndi cuma coona?

12 Ndipo ngati simunakhala okhulupirika ndi zace za wina, adzakupatsani inu ndani za inu eni?

13 Palibe mnyamata wa m'nyumba akhoza kukhala kapolo wa ambuye awiri; pakuti kapena adzamuda wina, nadzakonda winayo; kapena adzatsata wina, nadzapeputsa winayo. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa Cuma.

14 Koma Marisi, ndiwo okonda ndalama, anamva izi zonse; ndipo anamseka.

15 Ndipo anati kwa iwo, Inu ndinu odziyesera nokha olungama pamaso pa anthu; koma Mulungu azindikira mitima yanu; cifukwa ici cimene cikuzika mwa anthu ciri conyansa pamaso pa Mulungu.

16 Cilamulo ndi aneneci analipo kufikira pa Yohane; kuyambira pamenepo ulalikidwa Uthenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu, ndipo munthu ali yense akangamira kulowamo.

17 Kuti kumwamba ndi dziko lapansi zicoke nkwapafupi, koma kuti kalembo kakang'ono ka cilamulo kagwe nkwapatali.

18 Yense wakusudzula mkazi wace, nakwatira wina, acita cigololo; ndipo iye amene akwatira wosudzulidwayo, acita cigololo,

19 Ndipo panali munthu mwini cuma amabvala cibakuwa ndi nsaru yabafuta, nasekera, nadyerera masiku onse;

20 ndipo wopemphapempha wina, dzina lace Lazaro, adaikidwa pakhomo pace wodzala ndi zironda,

21 ndipo anafuna kukhuta ndi zakugwa pa gome la mwini cumayo; komatu agarunso anadza nanyambita zirondazace.

22 Ndipo kunali kuti wopemphayo adafa, ndi kuti anatengedwa iye ndi angelo kunka ku cifuwa ca Abrahamu; ndipo mwini cumayo adafanso, naikidwa m'manda.

23 Ndipo m'Hade anakweza maso ace, pokhala nao mazunzo, naona Abrahamu patali, ndi Lazaro m'cifuwa mwace.

24 Ndipo anakweza mau nati, Atate Abrahamu, mundicitire cifundo, mutome Lazaro, kuti abviike nsonga ya cala cace m'madzi, naziziritse lilime langa; pakuti ndizunzidwadi m'lawi ili la moto.

25 Koma Abrahamu anati, Mwana, kumbukila kuti unalandira zokoma zako pakukhala m'moyo iwe, momwemonso Lazaro zoipa; ndipo tsopano iye asangalatsidwa pano, koma iwe uzunzidwadi.

26 Ndipo pamwamba pa izi, pakati pa ife ndi inu pakhazikika phompho lalikuru, kotero kuti iwo akufuna kuoloka kucokera kuno kunka kwa inu sangathe, kapena kucokera kwanuko kuyambuka kudza kwa ife, sangathenso.

27 Koma anati, Pamenepo ndikupemphani, Atate, kuti mumtume ku nyumba ya atate wanga;

28 pakuti ndirinao abale asanu; awacitire umboni iwo kuti iwonso angadze ku malo ana a mazunzo.

29 Koma Abrahamu anati, Ali ndi Mose ndi aneneri; amvere iwo.

30 Koma anati, lai, Atate Abrahamu, komatu ngati wina akapita kwa iwo wocokera kwa akufa adzasandulika mtima.

31 Koma anati kwa iye, Ngati samvera Mose ndi aneneri, sadzakopeka mtima ngakhale wina akauka kwa akufa.

17

1 Ndipo anati kwa ophunzira ace, Sikutheka kuti zolakwitsa zisadze; koma tsoka iye amene adza nazo.

2 Kukolowekedwa mwala wamphero m'khosi mwace ndi kuponyedwa Iye m'nyanja nkwapafupi, koma kulakwitsa mmodzi wa ang'ono awa nkwapatali.

3 Kadzicenjerani nokha; akacimwa mbale wako umdzudzule; akalapa, umkhululukire.

4 Ndipo akakucimwira kasanu ndi kawiri pa tsiku lace, nakakutembenukira kasanu ndi kawiri ndi kunena, Ndalapa ine; uzimkhululukira.

5 Ndipo atumwi anati kwa Ambuye, Mutionjezere cikhulupiriro.

6 Koma Ambuye anati, Mukakhala naco cikhulupiriro ngati kambeu kampiru, mukanena kwa mtengo uwu wamkuyu, Uzulidwe, nuokedwe m'nyanja; ndipo ukadamvera inu.

7 Koma ndani mwa inu ali naye kapolo wolima, kapena woweta nkhosa, amene pobwera iye kucokera kumunda adzanena kwa iye, Lowa tsopano, khala pansi kudya;

8 wosanena naye makamaka, Undikonzere cakudya me, nudzimangire, nunditumikire kufikira ndadya ndi kumwa; ndipo nditatha ine udzadya nudzamwa iwe?

9 Kodi ayamika kapoloyocifukwa anacita zolamulidwa?

10 Cotero Inunso m'mene mutacita zonse anakulamulirani, Denani, Ife ndife akapolo opanda pace, tangocita zimene tayenera kuzicita.

11 Ndipo kunali, pakumuka ku Yerusalemu iye analikupita pakati pa Samariya ndi Galileya.

12 Ndipo m'mene analowa iye m'mudzi wina, anakomana naye amuna khumi akhate, amene anaima kutali;

13 ndipo iwo anakweza mau, nanena, Yesu, Mbuye, muticitire cifundo.

14 Ndipo pakuwaona anati kwa iwo, Pitani, kadzionetseni nokha kwa ansembe. Ndipo kunali, m'kumuka kwao, anakonzedwa.

15 Ndipo mmodzi wa iwo, pakuona kuti anaciritsidwa, anabwerera m'mbuyo, nalemekeza Mulungu ndi mau akuru;

16 ndipo anagwa nkhope yace pansi ku mapazi ace, namyamika iye; ndipo anali Msamariya ameneyo.

17 Ndipo Yesu anayankha nati, Kodi sanakonzedwa khumi? koma ali kuti asanu ndi anai aja?

18 Akubwera kulemekeza Mulungu sanapezeka mmodzi kodi, koma mlendo uyu?

19 Ndipo anati kwa iye, Nyamuka, nupite; cikhulupiriro cako cakupulumutsa iwe.

20 Ndipo pamene Afarisi anamfunsa iye, kuti, Ufumu wa Mulungu ukudza liti, anawayarikha, nati, Ufumu wa Mulungu sukudza ndi maonekedwe;

21 ndipo sadzanena, Taonani uwu, kapena uwo! Pakuti, taonani, Ufumu wa Mulungu uli m'kati mwa inu.

22 Ndipo anati kwa ophunzira ace, Adzadza masiku, amene mudzakhumba kuona limodzi la masiku a Mwana wa munthu, koma simudzaliona.

23 Ndipo adzanena ndi inu, Taonani ilo! taonani ili! musacoka kapena kuwatsata;

24 pakuti monga mphezi ing'anipa kucokera kwina pansi pa thambo, niunikira kufikira kwina pansi pa thambo, kotero adzakhala Mwana wa munthu m'tsiku lace.

25 Koma ayenera athange wamva zowawa zambiri nakanizidwe ndi mbadwo uno.

26 Ndipo monga kunakhala masiku a Nowa, momwemo kudzakhalanso masiku a Mwana wa munthu.

27 Anadya, anamwa, anakwatira, anakwatiwa, kufikira tsiku lija Nowa analowa m'cingalawa, ndipo cinadza cigumula, niciwaononga onsewo.

28 Monga momwenso kunakhala masiku a Loti; anadya, anamwa, anagula, anagulitsa, anabzala, anamanga nyumba;

29 koma tsiku limene Loti anaturuka m'Sodoma udabvumba mota ndi sulfure zocokera kumwamba, ndipo zinawaononga onsewo;

30 momwemo kudzakhala tsiku lakubvumbuluka Mwana wa munthu.

31 Tsikulo iye amene adzakhala pamwamba pa chindwi, ndi akatundu ace m'nyumba, asatsike kuwatenga; ndipo iye amene ali m'munda modzimodzi asabwere ku zace za m'mbuyo.

32 Kumbukilani mkazi wa Loti,

33 iye ali yense akafuna kusunga moyo wace adzautaya, koma iye ali yense akautaya, adzausunga.

34 Ndinena ndi inu, usiku womwewo adzakhala awiri pa kama mmodzi; mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa.

35 Padzakhala akazi awiri akupera pamodzi, mmodzi adzatengedwa, ndi wina adzasiyidwa. [

36 ]

37 Ndipo anayankha nanena kwa iye, Kuti, Ambuye? Ndipo anati kwa iwo, Pamene pali mtembo, pomweponso miimba idzasonkhanidwa.

18

1 Ndipo anawanenera fanizo lakuti ayenera iwo kupemphera nthawi zonse, osafoka mtima;

2 nanena, M'mudzi mwakuti munali woweruza wosaopa Mulungu, ndi wosasamala munthu.

3 Ndipo m'mudzimo munali mkazi wamasiye; ndipo anadza kwa iye nanena, Mundiweruzire mlandu pa wotsutsana nane.

4 Ndipo sanafuna nthawi; koma bwino bwino anati mwa yekha, Ndingakhale sindiopa Mulungu kapena kusamala munthu;

5 koma cifukwa ca kundibvuta ine mkazi wamasiye amene ndidzamweruzira mlandu, kuti angandilemetse ndi kudzaidza kwace.

6 Ndipo Ambuye anati, Tamverani conena woweruza wosalungama.

7 Ndipo kodi Mulungu sadzacitira cilungamo osankhidwa ace akumuitana usana ndi usiku, popeza aleza nao mtima?

8 Ndinena ndi inu, adzawacitira cilungamo posacedwa. Koma Mwana wa munthu pakudza Iye, vadzapeza cikhulupiriro pa dziko lapansi kodi?

9 Ndipo anatinso kwa ena amene anadzikhulupirira mwa iwo okha kuti ali olungama, napeputsa onse ena, fanizo ili,

10 Anthu awiri anakwera kunka kukacisi kukapemphera; winayo Mfarisi ndi mnzace wamsonkho.

11 Mfarisiyo anaimirira napemphera izi mwa yekha, Mulungu, ndikuyamikani kuti sindiri monga anthu onse ena, opambapamba, osalungama, acigololo, kapenanso monga wamsonkho uyu;

12 ndisala cakudya kawiri sabata limodzi; ndipereka limodzi lamagawo khumi la zonse ndiri nazo.

13 Koma wamsonkhoyo alikuima patali sanafuna kungakhale kukweza maso kumwamba, komatu anadziguguda pacifuwa pace nanena, Mulungu, mundicitire cifundo, ine wocimwa.

14 Ndinena ndi inu, anatsikira kunyumba kwace woyesedwa wolungama uyutu, wosati uja ai; pakuti yense wakudzikuza yekha adzacepetsedwa; koma wodzicepetsa yekha adzakulitsidwa.

15 Ndipo anadzanao kwa iye ana amakanda kuti awakbudze; koma pamene ophunzira anaona, anawadzudzula.

16 Koma Yesu anawaitana, nanena, Lolani ana adze kwa Ine, ndipo musawaletse; pakuti Ufumu wa Mulungu uti wa otere.

17 Indetu ndinena kwa inu, Ali yense wosalandira Ufumu wa Mulungu ngati mwana, sadzalowamo ndithu.

18 Ndipo mkuru wina anamfunsa iye, nanena, Mphunzitsi wabwino, ndizicita ciani, kuti ndilowe moyo wosatha?

19 Koma Yesu anati kwa iye, Undicha Ine wabwino bwanji? palibe wabwino, koma mmodzi, ndiye Mulungu.

20 Udziwa malamulo. Usacite cigololo, Usaphe, Usabe, Usacite umboni wonama, Lemekeza atate wako ndi amako.

21 Koma anati, Izi zonse ndazisunga kuyambira ubwana wanga.

22 Koma m'mene Yesu anamva, anati kwa iye, Usowa cinthu cimodzi: gulitsa ziri zonse uli nazo, nugawire osauka; ndipo udzakhala naco cuma ceni ceni m'Mwamba; ndipo ukadze kuno, unditsate Ine.

23 Koma pakumva izi anagwidwa naco cisoni cambiri; pakuti anali mwini cuma cambiri.

24 Ndipo Yesu pomuona iye anati, Ha! nkubvutika nanga kwa anthu eni cuma kulowa Ufumu wa Mulungu!

25 Pakuti nkwapafupi kwa ngamila apyole diso la singano koma kwa munthu mwini cuma, kulowa Ufumu wa Mulungu nkwapatali.

26 Koma akumvawo anati, Tsono ndani angathe kupulumutsidwa?

27 Koma iye anati, Zinthu zosatheka ndi anthu zitheka ndi Mulungu.

28 Ndipo Petro anati, Taonani ife tasiya zathu za ife eni, ndipo takutsatani Inu.

29 Koma anati kwa iwo, Indetu ndinena kwa inu, Palibe munthu wasiya nyumba, kapena mkazi, kapena abale, kapena akumbala, kapena ana, cifukwa ca Ufumu wa Mulungu,

30 koma adzalandira zobwezedwa koposatu m'nthawi yino; ndipo m'nthawi irinkudza moyo wosatha.

31 Ndipo anadzitengera khumi ndi awiriwo, nati kwa iwo, Taonani, tikwera kunkaku Yerusalemu, ndipo zidzakwaniritsidwa kwa Mwana wa munthu zonse zolembedwa ndi aneneri.

32 Pakuti adzampereka kwa amitundu, nadzamseka, nadzamcitira cipongwe, nadzamthira malobvu; ndipo atamkwapula adzamupha iye;

33 ndipo tsiku lacitatu adzauka.

34 Ndipo sanadziwitsa kanthu ka izi; ndi mau awa adawabisikira, ndipo sanazindikira zonenedwazo.

35 Ndipo kunali, pamene anayandikira ku Yeriko, msaona wina anakhala m'mbali mwa njira, napemphapempha;

36 ndipo pakumva khamu la anthu alinkupita, anafunsa, ici nciani?

37 Ndipo anamuuza iye, kuti, Yesu Mnazarayo alinkupita.

38 Ndipo anapfuula, nanena, Yesu, Mwana wa Davine, mundicitire cifundo.

39 Ndipo iwo akutsogolera anamdzudzula iye, kuti akhale cete; koma iye anapfuulitsa cipfuulire, Mwana wa Davine, mundicitire cifundo.

40 Ndipo Yesu anaima, nalamulira kuti abwere naye kwa iye: ndipo m'mene adafika pafupi, anamfunsa iye,

41 Of una ndikucitire ciani? Ndipo anati, Ambuye, kuti ndipenyenso.

42 Ndipo Yesu anati kwa iye, Penyanso: cikhulupiriro cako cakupulumutsa iwe.

43 Ndipo pomwepo anapenyanso, namtsata iye, ndi kulemekeza Mulungu: ndipo anthu onse pakuona, anacitira Mulungu mayamiko.

19

1 Ndipo analowa, napyola pa Yeriko. Ndipo taonani, mwamuna wochedwa dzina lace Zakeyu;

2 ndipo Iye anali mkulu wa amisonkho, nali wacuma.

3 Ndipo anafuna kuona Yesu ndiye uti, ndipo sana the, cifukwa ca khamulo, pakuti anali wamfupi msinkhu.

4 Ndipo anathamanga, natsogola, nakwera mumkuyu kukamuona iye; pakuti anati apite njira yomweyi.

5 Ndipo m'mene anadza pamalopo Yesu anakweza maso nati kwa iye, Zakeyu, fulumira, nutsike; pakuti lero ndiyenera kukhala m'nyumba mwako.

6 Ndipo anafulumira, natsika, namlandira iye wokondwera.

7 Ndipo m'mene anaciona anadandaula onse, nanena, Analowa amcereze munthu ali wocimwa.

8 Ndipo Zakeyu anaimirira nati kwa Ambuye, Taonani, Ambuye, gawo limodzi la zanga zonse zogawika pakati ndipatsa osauka; ndipo ngati ndalanda kanthu kwa munthu monyenga, ndimbwezera kanai.

9 Ndipo Yesu anati kwa iye, Lero cipulumutso cagwera nyumba iyi, popeza iyenso ndiye mwana wa Abrahamu.

10 Pakuti Mwana wa munthu anadza kufunafuna ndi kupulumutsa, cotayikaco.

11 Ndipo pakumva izi iwo, iye anaonjeza nanena fanizo, cifukwa anali iye pafupi pa Yerusalemu, ndipo iwo anayesa kuti Ufumu wa Mulungu ukuti uonekere pomwepo.

12 Pamenepo: anati, Munthu wa pfuko lomveka ananka ku dziko lakutali, kudzilandirira yekha ufumu, ndi kubwerako.

13 Ndipo anaitana akapolo ace khumi, nawapatsa iwo ndalama khumi, nati kwa iwo, Cita nazoni malonda kufikira ndibweranso.

14 Koma mfulu za pamudzi pace zinamuda, nizituma akazembe amtsate m'mbuyo ndi kunena, Ife sitifuna munthuyu akhale mfumu yathu.

15 Ndipo kunali, pakubwera iye, atalandira ufumuwo, anati aitanidwe kwa iye akapolo aja, amene adawapatsa ndalamazo, kuti adziwe umo anapindulira pocita malonda.

16 Ndipo anafika woyamba, nanena, Mbuye ndalama yanu inacita nionjeza ndalama khumi.

17 Ndipo anati kwa iye, Cabwino, kapolo wabwino iwe; popeza unakhala wokhulupirika m'cacing'onong'ono, khala nao ulamuliro pa midzi khumi.

18 Ndipo anadza waciwiri, nanena, Mbuye, ndalama yanu yapindula ndalama zisanu.

19 Ndipo anati kwa iyenso, Khala iwenso woweruza midzi isanu.

20 Ndipo wina anadza, nanena, Mbuye, taonani, siyi ndalama yanu, ndaisunga m'kansaru;

21 pakuti ndinakuopani, popeza inu ndinu munthu wouma mtima: munyamula cimene simunaciika pansi, mututa cimene simunacifesa.

22 Ananena kwa iye, Pakamwa pako ndikuweruza, kapolo woipa iwe. Unadziwa kuti ine ndine munthu wouma mtima, wonyamula cimene sindinaciika, ndi wotuta cimene sindinacifesa;

23 ndipo sunapereka bwanji ndalama yanga pokongoletsa, ndipo ine pakudza ndikadaitenga ndi phindu lace?

24 Ndipo anati kwa iwo akuimirirapo, Mcotsereni ndalamayo, nimuipatse kwa iye wakukhala nazo ndalama khumi.

25 Ndipo anati kwa iye, Mbuye, ali nazo ndalama khumi.

26 Ndinena ndi inu, kuti kwa yense wakukhala naco kudzapatsidwa; koma kwa iye amene alibe kanthu, cingakhale cimene ali naco cidzacotsedwa.

27 Koma adani anga aja osafuna kuti ndidzakhala mfumu yao, bwerani cao kuno, nimuwaphe pamaso panga,

28 Ndipo m'mene adanena izi anawatsogolera nakwera ku Yerusalemu.

29 Ndipo kunali, m'mene anayandikira ku Betefage ndi Betaniya, pa phiri lochedwa la Azitona, anatuma awiri a ophunzira,

30 nati, Mukani ku mudzi uli pandunji panu; m'menemo, polowa, mudzapeza mwana wa buru womangidwa, pamenepo palibe munthu anakwerapo nthawi iri yonse; mummasule iye nimumtenge.

31 Ndipomunthuakati kwa inu, Mummasuliranji? mudzatero naye, Ambuye amfuna iye.

32 Ndipo anacoka otumidwawo, napeza monga adanena kwa iwo.

33 Ndipo pamene anamasula mwana wa buru, eni ace anati kwa iwo, Mumasuliranji mwana wa buru?

34 Ndipo anati, Ambuye amfuna iye.

35 Ndipo anadzanave kwa Yesu; ndipo anayalika zobvala zao pa mwana wa buruyo, nakwezapo Yesu.

36 Ndipo pakupita iye, anayala zobvala zao m'njira.

37 Ndipo pakuyandikira iye tsono potsetsereka pace pa phiri la Azitona, unyinji wonse wa ophunzira anayamba kukondwera ndi kuyamika Mulungu ndi mau akuru, cifukwa ca nchito zonse zamphamvu anaziona;

38 nanena, Wolemekezeka Mfumuyo ikudza m'dzina la Ambuye; mtendere m'Mwamba, ndi ulemerero m'Mwambamwamba.

39 Ndipo Afarisi ena a m'khamu la anthu anati kwa iye, Mphunzitsi, dzudzulani ophunzira anu.

40 Ndipo anayankha nati, Ndinena ndi inu, ngati awa akhala cete miyala idzapfuula.

41 Ndipo m'meneanayandikira, anaona mudziwo naulirira,

42 nanena, Ukadazindikira tsiku ili, inde iwetu zinthu za mtendere! koma tsopano zibisika pamaso pako.

43 Pakuti masiku adzakudzera, ndipo adani ako adzakuzingira linga, nadzakuzungulira iwe kwete, nadzakutsekereza ponsepo;

44 ndipo adzakupasula iwe, ndi ana ako mwa iwe; ndipo sadzasiya mwa iwe mwala wina pa mwala unzace; popeza sunazindikira nyengo, ya mayang'aniridwe ako.

45 Ndipo analowa m'Kacisi, nayamba kuturutsa iwo akugulitsa malonda, nanena nao,

46 Kwalembedwa, Ndipo nyumba yanga idzakhala nyumba yakupemphera; koma inu mwaiyesa iyo phanga la acifwamba.

47 Ndipo analikuphunzitsa m'Kacisi tsiku ndi tsiku. Koma ansembe akulu, ndi alembi ndi akulu a anthu anafunafuna kumuononga iye;

48 ndipo sanapeza cimene akacita; pakuti anthu onse anamlendewera iye kuti amve.

20

1 Ndipo kunali lina la masiku awo m'mene iye analikuphunzitsa anthu m'Kacisi, ndi kulalikira Uthenga Wabwino, adamdzera ansembe akulu ndi alembi pamodzi ndi akulu;

2 ndipo anati, nanena naye, Mutiuze mucita in ndi ulamuliro wotani? Kapena ndani iye amene anakupatsani ulamuliro umene?

3 Ndipo anayankha, nati kwa iwo, Ndidzakufunsani mau Inenso; mundiuze:

4 Ubatizo wa Yohane unacokera Kumwamba kodi, kapena kwa anthu?

5 Ndipo anatsutsana mwa okha, nanena, Ngati tinena ucokera Kumwamba; adzati, Simunamkhulupirira cifukwa ninji?

6 ndiponso, tikanena, Ucokera kwa anthu; anthu onse adzatiponya miyala: pakuti akopeka mtima, kuti Yohane ali mneneri.

7 Ndipo anayankha kuti sadziwa kumene ucokera.

8 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ndingakhale Inenso sindikuuzani ulamuliro umene ndicita nao zinthu izi.

9 Ndipo iye anayamba kunena kwa anthu fanizo ili: Munthu analima munda wamphesa, naukongoletsa kwa olima munda, nanka ku dziko lina, nagonerako nthawi yaikuru.

10 Ndipo pa nyengo ya zipatso anatumiza kapolo wace kwa olima mundawo, kuti ampatseko cipatso ca mundawo; koma olimawo anampanda, nambweza wopanda kanthu.

11 Ndipo anatumizanso kapolo wina; ndipo iyenso anampanda, namcitira cipongwe, nambweza, wopanda kanthu.

12 Ndipo anatumizanso wina wacitatu; ndipo iyenso anamlasa, namtaya kunja.

13 Ndipo mwini mundawo anati, Ndidzacita ciani? Ndidzatuma mwana wanga amene ndikondana naye; kapena akamcitira iye ulemu.

14 Koma olimawo, pamene anamuona, anauzana wina ndi mnzace, nati, Uyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe, kuti colowa cace cikhale cathu.

15 Ndipo anamponya kunja kwa mundawo, namupha, Pamenepo mwini munda wamphesawo adzawacitira ciani?

16 iye adzafika nadzaononga olima munda aja, nadzapatsa munda kwa ena. Ndipo pamene iwo anamva, anati, Musatero iail

17 Koma iye anawapenyetsa iwo, nati, Nciani ici cinalembedwa, Mwala umene anaukana omanga nyumba, Womwewu unakhala mutu wa pangondya.

18 Munthu yense wakugwa pa mwala uwu, adzaphwanyika; koma iye amene udzamgwera, udzamupha.

19 Ndipo alembi ndi ansembe akuru anafunafuna kumgwira ndi manja nthawi yomweyo; ndipo anaopa anthu; pakuti anazindikira kuti ananenera pa iwo fanizo ili.

20 Ndipo anamyang'anira, natumiza ozonda, amene anadzionetsera ngati olungama mtima, kuti akamkole pa mau ace, kotero kuti akampereke iye ku ukulu ndi ulamuliro wa kazembe.

21 Ndipo anamfunsa iye, nanena, Mphunzitisi, ife tidziwa kuti munena ndi kuphunzitsa kolunjika, ndi kusasamalira nkhope ya munthu, koma muphunzitsa njira ya Mulungu koonadi;

22 kodi kuloledwa kupereka msonkho kwa Kaisara, kapena iai?

23 Koma iye anazindikira cinyengo cao, nati kwa iwo,

24 Tandionetsani Ine rupiya latheka. Cithunzithunzi ndi colemba cace nca yani? Anati iwo, Ca Kaisara.

25 Ndipo iye anati kwa iwo, Cifukwa cace perekani kwa Kaisara zace za Kaisara, ndi kwa Mulungu zace za Mulungu.

26 Ndipo sanakhoza kugwira mauwo pamaso pa anthu; ndipo anazizwa ndi kuyankha kwace, nakhala cete.

27 Ndipo anadza kwa iye Asaduki ena, amene amanena kuti palibe kuuka kwa akufa; ndipo anamfunsa iye,

28 nanena, Mphunzitsi, Mose anatilembera ire, kuti mbale wace wa munthu akafa, wokhala ndi mkazi, ndipo ali be mwana iye, mbale wace adzakwatira mkaziyo, nadzamuukitsira mbale wace mbeu.

29 Tsono panali abale asanu ndi awiri; ndipo woyamba anakwatira mkazi, nafa wopanda mwana;

30 ndipo waciwiri,

31 ndi wacitatu anamtenga mkaziyo; ndipo coteronso asanu ndi awiri onse, sanasiya mwana, namwalira.

32 Pomarizira anamwaliranso mkaziyo.

33 Potero m'kuuka iye adzakhala mkazi wa yani wa iwo? pakuti asanu ndi awiriwo adamkwatira iye.

34 Ndipo Yesu anati kwa iwo, Ana a dziko lapansi akwatira nakwatiwa:

35 koma iwo akuyesedwa oyenera kufikira dzikolijalo, ndi kuuka kwa akufa, sakwatira kapena kukwatiwa.

36 Pakuti sangathe kufanso nthawi zonse; pakuti afanafana ndi angelo; ndipo ali ana a Mulungu, popeza akhala ana a kuuka kwa akufa.

37 Koma za kuti anthu akufa auka, anasonyeza ngakhale Mose, pa Citsamba cija, pamene iye amchulira Ambuye, Mulungu wa Abrahamu, ndi Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.

38 Ndipo iye sakhala Mulungu wa akufa, koma wa amoyo: pakuti anthu onse akhala ndi moyo kwa iye.

39 Ndipo alembi ena anayankha nati, Mphunzitsi, mwanena bwino.

40 Pakuti sanalimbanso mtima kumfunsa iye kanthu kena.

41 Koma iye anati kwa iwo, Amanena bwanji kuti Kristuyo ndiye mwana wa Davine?

42 Pakuti Davine yekha anena m'buku la Masalmo, Ambuye ananena kwa Ambuye wanga, Ukhale pa dzanja langa lamanja,

43 Kufikira Ine ndikaika adani ako pansi pa mapazi ako.

44 Cotero Davine anamchula iye Ambuye, ndipo nanga ali mwana wace bwanji?

45 Ndipo pamene anthu onse anallinkumva iye, anati kwa ophunzira,

46 Cenjerani nao alembi, amene afuna kuyendayenda obvala miinjiro, nakonda kulankhulidwa m'misika, ndi mipando yaulemu m'sunagoge, ndi malo aulemu pamapwando;

47 amene aononga nyumba za akazi amasiye, ndipo monyenga acita mai pemphero atali; amenewo adzalandira kulanga koposa.

21

1 Ndipo Yesu anakweza maso, naona anthu eni cuma alikuika zopereka zao mosungiramo ndalama.

2 Ndipo anaona mkazi wina wamasiye waumphawi alikuika momwemo timakobiri tiwiri.

3 Ndipo iye anati, Zoonadi ndinena kwa inu, wamasiye uyu waumphawi anaikamo koposa onse;

4 pakuti onse amenewa anaika mwa unyinji wao pa zoperekazo; koma iye mwa kusowa kwace anaikamo za moyo wace, zonse anali nazo.

5 Ndipo pamene ena analikunena za Kacisiyo, kuti anakonzeka ndi miyala yokoma ndi zopereka, anati iye,

6 Zinthu izi muziona, adzafika masiku, pamenepo sudzasiyidwa pano mwala pa mwala unzace, umene sudzagwetsedwa.

7 Ndipo iwo anamfunsa iye, nati, Mphunzitsi, nanga zinthu izi zidzaoneka liti? ndipo cizindikilo ndi cianipamene izi ziti zicitike?

8 Ndipo iye anati, Yang'anirani musasoceretsedwe; pakuti ambiri adzadza m'dzina langa, nadzanena, Ndine amene; ndipo, Nthawi yayandikira; musawatsate pambuyo pao.

9 Ndipo pamene mudzamva za nkhondo ndi mapanduko, musaopsedwa; pakuti ziyenera izi ziyambe kucitika; koma mathedwe sakhala pomwepo.

10 Pamenepo ananena nao, Mtundu wa anthu udzaukira pa mtundu wina, ndipo ufumu pa ufumu wina:

11 ndipo kudzakhala zibvomezi zazikuru, ndi njala ndi miliri m'malo akutiakuti, ndipo kudzakhala zoopsya ndi zizindikilo zazikuru zakumwamba.

12 Koma zisanacitike izi, anthu adzakuthirani manja, nadzakuzunzani, nadzapereka inu ku masunagoge ndi ndende, nadzamuka nanu kwa mafumu ndi akazembe, cifukwa ca dzina langa.

13 Kudzakhala kwa inu ngati umboni.

14 Cifukwa cace tsimikizani mumtima mwanu, kuti usanafike mlandu musalingirire cimene mudzayankha.

15 Pakuti Ine ndidzakupatsani inu kamwa ndi nzeru, zimene adani anu onse sadzatha kuzikana kapena kuzitsutsa.

16 Koma mudzaperekedwa ngakhale ndi akukubalani, ndi abale, ndi a pfuko lanu, ndi abwenzi anu; ndipo ena a inu adzakuphani,

17 Ndipo anthu onse adzadana ndi inu cifukwa ca dzina langa.

18 Ndipo silidzaonongeka tsitsi limodzi la pamutu panu.

19 Mudzakhala nao moyo wanu m'cipiriro.

20 Koma pamene pali ponse mudzaona Yerusalemu atazingidwa ndi magulu a ankhondo, zindikirani pamenepo kuti cipululutso cace cayandikira.

21 Pamenepo iwo ali m'Yudeya athawire kumapiri, ndi iwo ali m'kati mwa uwo aturuke, ndi iwo ali kumiraga asalowemo.

22 Cifukwa amenewa ndi masiku akubwezera, kuti zonse zidalembedwa zicitike.

23 Koma tsoka iwo akukhala ndi pakati, ndi iwo akuyamwitsa ana masiku awo! pakuti padzakhala cisauko cacikuru padziko, ndi mkwiyo pa anthu awa.

24 Ndipo adzagwa ndi lupanga lakuthwa, nadzagwidwa ndende kunka ku mitundu yonse ya anthu; ndipo mapazi a anthu akunja adzapondereza kufikira kuti nthawi zao za anthu akunja zakwanira.

25 Ndipo kudzakhala zizindikilo pa dzuwa ndi mwezi ndi nyenyezi; ndi pa dziko lapansi cisauko ca mitundu ya anthu, alikuthedwa nzeru pa mkukumo wace wa nyanja ndi mafunde ace;

26 anthu akukomoka ndi mantha, ndi kuyembekeeera zinthu zirinkudza ku dziko lapansi;

27 pakuti mphamvu zakumwamba zidzagwedezeka. Ndipo pamenepo adzaona Mwana wa munthu alinkudza mu mtambo ndi mphamvu ndi ulemerero waukuru.

28 Komapoyamba kucitika izi weramukani, tukulani mitu yanu; cifukwa ciomboledwe canu cayandikira.

29 Ndipo ananena nao fanizo; Onani mkuyu, ndi mitengo yonse:

30 pamene iphukira, muipenya nimuzindikira pa nokha kuti dzinja liri pafupi pomwepo.

31 Inde cotero inunso, pakuona zinthu izi zirikucitika, zindikirani kuti Ufumu wa Mulungu uli pafupi.

32 Indetu ndinena ndinu, Mbadwo uno sudzapitirira, kufikira zonse zitacitika.

33 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzapita; koma mau anga sadzapita.

34 Koma mudziyang'anire nokha, kuti kapena mitima yanu ingalemetsedwe ndi madyaidya ndi kuledzera, ndi zosamalira za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingafikire inu modzidzimutsa ngati msampha;

35 pakuti Iidzatero ndi kufikira anthu onse akukhala pankhope pa dziko lonse lapansi.

36 Koma inu dikirani nyengo zonse ndi kupemphera, kutimukalimbike kupulumuka zonse zimene zidzacitika, ndi kuimirira pamaso pa Mwana wa munthu.

37 Ndipo usana uli wonse iye analikuphunzitsa m'Kacisi; ndi usiku uli wonse anaturuka, nagona pa phiri lochedwa la Azitona.

38 Ndipo anthu onse analawira mamawa kudza kwa iye kuKacisi kudzamvera Iye.

22

1 Ndipo phwando la mikate yopanda cotupitsa linayandikira, ndilo lochedwa Paskha.

2 Ndipo ansembe akuru ndi alembi anafunafuna maphedwe ace pakuti anaopa anthuwoo.

3 Ndipo Satana analowa m'Yudase wonenedwa Isikariote, amene anawerengedwa mmodzi wa khumi ndi awiriwo,

4 Ndipo iye anacoka, nalankhulana ndi ansembe akulu ndi akazembe mompereka iye kwa iwo.

5 Ndipo anakondwera, napangana naye kumpatsa ndalama.

6 Ndipo iye anabvomera, nafunafuna nthawi yabwino yakumpereka iye kwa iwo, pakalibe khamu la anthu.

7 Ndipo tsiku la mikate yopanda cotupitsa linafika, limene inayenera kuphedwa nsembe ya Paskha.

8 Ndipo iye anatumiza Petro ndi Yohane, nati, Pitanimutikonzere ife Paskha, kuti tidye.

9 Ndipo iwo ananena naye, Mufuna tikakonzere kuti?

10 Ndipo iye anati kwa iwo, Onani, mutalowa m'mudzi, adzakomana ndinu munthu alikusenza mtsuko wa madzi; mumtsate ameneyo kunyumba kumene akalowako iye.

11 Ndipo mukanene kwa mwini nyumbayo, Mphunzitsi anena nawe, Cipinda ca alendo ciri kuti, m'mene ndikadye Paskha pamodzi ndi ophunzira anga?

12 Ndipo iyeyo adzakuonetsani cipinda cacikuru capamwamba, cokonzeka; mukakonzere kumeneko.

13 Ndipo anapita iwo, napeza monga adatero nao; ndipo anakonza Paskha.

14 Ndipo itadza nthawi yace, iye anakhala pacakudya, ndi ophunzira pamodzi ndi iye.

15 Ndipo anati kwa iwo, Ndinalakalaka ndithu kudya Paskha uwu pamodzi ndinu, ndisanayambe kusautsidwa;

16 pakuti ndinena ndi inu, sindidzadya kufikira udzakwaniridwa mu Ufumu wa Mulungu.

17 Ndipo analandira cikho, ndipo pamene adayamika, anati, Landirani ici, mucigawane mwa inu nokha;

18 pakuti ndinena kwa inu, kuyambira tsopano Ine sindidzamwako cipatso ca mpesa, kufikira Ufumu wa Mulungu udzafika.

19 Ndipo m'mene adatenga mkate, nayamika, anaunyema, nawapatsa, nanena, ici ndi thupi langa lopatsidwa cifukwa ca inu; citani ici cikumbukilo canga.

20 Ndipo coteronso cikho, atatha mgonero, nanena, Cikho ici ndi pangano latsopano m'mwazi wanga wothiridwa cifukwa ca inu.

21 Koma onani, dzanja lace la iye amene adzandipereka ali pagome pano pamodzi ndi Ine.

22 Pakuti Mwana wa munthu amukatu, monga kunaikidwiratu; koma tsoka munthuyo amene ampereka!

23 Ndipo anayamba kufunsana mwa iwo okha, ndiye yani mwa iwo amene adzacita ici.

24 Ndipo kunakhala kutsutsana mwa iwo, ndani wa iwo ayesedwe wamkuru.

25 Ndipo anati kwa iwo, Mafumu a anthu a mitundu awacitira ufumu; ndipo iwo amene awacitira ulamuliro anenedwa, Ocitira zabwino.

26 Koma sipadzatero ndi inu; komatu iye ali wamkuru mwa inu, akhale ngati wamng'ono; ndi iye ali woyamba, akhale ngati wotumikira.

27 Pakuti wamkuru ndani, iye wakuseama pacakudya kapena wakutumikirapo? si ndiye wakuseama pacakudya kodi? koma Ine ndiri pakati pa inu monga ngati wotumikira.

28 Koma inu ndinuamene munakhala ndi Ine cikhalire m'mayesero anga;

29 ndipo Ine ndikuikirani ufumu, monganso Atate wanga anandiikira Ine, kuti mukadye ndi kumwa kugome kwanga mu Ufumu wanga;

30 ndipo mudzakhala pa mipando yacifumu ndi kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israyeli.

31 Simoni, Simoni, taona, Satana anafunsa akutengeni kuti akupeteni ngati tirigu;

32 koma ndinakupempherera kuti cikhulupiriro cako cingazime; ndipo iwe, pamene watembenuka ukhazikitse abale ako.

33 Ndipo anati kwa iye, Ambuye, ndiripo ndikapite ndi Inu kundende ndikuimfa.

34 Ndipo iye anati, Ndikuuza iwe, Petro, sadzalira tambala lero lino kufikira udzakana katatu kuti sundidziwa Ine.

35 Ndipo anati kwa iwo, Pamene ndinakutumizani opanda thumba la ndalama, ndi thumba la kamba, ndi nsapato, munasowa kanthu kodi? Anati iwo, Iai.

36 Ndipo anati kwaiwo, Koma tsopano, iye amene ali ndi thumba la ndalama, alitenge, ndi thumba la kamba lomwe; ndipo amene alibe, agulitse copfunda cace, nagule lupanga,

37 Pakuti ndinena ndi inu, cimene cidalembedwa ciyenera kukwanitsidwa mwa Ine, Ndipo anawerengedwa ndi anthu opanda lamulo; pakuti izi za kwa Ine ziri naco cimariziro.

38 Ndipo iwo anati, Ambuye, taonani, malupanga awir siwa. Ndipo anati kwa iwo, Cakwa nira.

39 Ndipo iye anaturuka, napita monga adafucita, ku phiri la Azitona ndi ophunzira anamtsata iye.

40 Ndipo pofika pomwepo, anati kwa iwo, Pempherani kuti mungalowe m'kuyesedwa.

41 Ndipo anapatukana nao kutalika kwace ngan kuponya mwala, nagwada pansi napemphera,

42 nati, Atate, mukafuna Inu, cotsani cikho ici pa Ine; koma si kufuna kwanga ai, komatu kwanu kucitike.

43 Ndipo anamuonekera iye 1 mngelo wa Kumwamba namlimbitsa iye.

44 Ndipo 2 pokhala iye m'cipsinjo mtima anapemphera kolimba koposa ndithu: ndi thukuta lace linakhala ngati madontho akuru a mwazi alinkugwa pansi.

45 Ndipo pamene ananyamuka pakupemphera anadza kwa ophunzira, nawapeza ali m'tulo ndi cisoni,

46 ndipo anati kwa iwo, Mugoneranji? Ukani, 3 pempherani kuti mungalowe m'kuyesedwa.

47 Pamene iye anali cilankhulire, taonani, khamu la anthu, ndipo iye wochedwa Yudase, mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anawatsogolera; nayandikira Yesu kumpsompsona iye.

48 Koma Yesu anati kwa iye, Yudase, ulikupereka Mwana wa munthu ndi cimpsompsono kodi?

49 Ndipo m'mene iwo akumzinga iye anaona cimene citi cicitike, anati, Ambuye, tidzakantha ndi lupanga kodi?

50 Ndipo wina wa iwo 4 anakantha kapolo wa mkuru wa ansembe, namdula khutu lace lamanja.

51 Koma Yesu anayankha nati, Lolani kufikira kumene. Ndipo anakhudza khutu lace, namciritsa.

52 Ndipo 5 Yesu anati kwa ansembe akulu ndi akapitao a Kacisi, ndi akuru, amene anadza kumgwira iye, Munaturuka ndi malupanga ndi mikunkhu kodi monga ngati kugwira wacifwamba?

53 Masiku onse, pamene ndinali ndi inu m'Kacisi, simunatansa manja anu kundigwira: koma 6 nyengo yino ndi yanu, ndipo ulamuliro wa mdima ndi wanu.

54 Ndipo 7 pamenepo anamgwira iye, napita naye, nalowa m'nyumba ya mkulu wa ansembe. Koma Petro anatsata kutari.

55 Ndipo 8 pamene adasonkha mota m'kati mwa bwalo, nakhala pansi pamodzi, Petro anakhala pakati pao.

56 Ndipo mdzakazi anamuona iye alikukhala m'kuwala kwace kwa moto, nampenyetsa iye, nati, Munthu uyunso anali naye.

57 Koma anakana, nati, Mkaziwe, sindimdziwa iye.

58 Ndipo 9 popita kamphindi, anamuona wina, nati, Iwenso uli mmodzi wa awo. Koma Petro anati, Munthu iwe, sindine.

59 Ndipo 10 patapita ngati ora limodzi, wina ananenetsa, kuti, Zoonadi, munthu uyunso anali naye, pakuti ndiye Mgalileya.

60 Koma Petro anati, Munthu iwe, sindidziwa cimene ucinena, Ndipo pomwepo, iye ali cilankhulire, tambala analira.

61 Ndipo Ambuye anapotoloka, nayang'ana Petro. Ndipo 11 Petra anakumbukila mau a Ambuye, kuti anati kwa iye, 12 Asanalire tambala lero lino, udzandikana Ine katatu.

62 Ndipo anaturuka, nalira misozi ndi kuwawa mtima.

63 Ndipo amuna amene analikusunga Yesu anamnyoza iye, nampanda.

64 Ndipo anamkulunga iye m'maso, namfunsa, nati, Talota; anakupanda Iwe ndani?

65 Ndipo zambiri zina anamnenera iye, namcitira mwano.

66 Ndipo 13 pamene kunaca, bungwe la akuru a anthu linasonkhana, ndiwo ansembe akuru ndi alembi; ndipo anapita naye ku bwalo lao, nanena, 14 Ngati uli Kristu, utiuze.

67 Ndipo anati kwa iwo, Ndikakuuzani, simudzabvomereza;

68 ndipo ndikakufunsani kanthu, simudzayankha.

69 Koma 15 kuyambira tsopano Mwana wa munthu adzakhala pa dzanja lamanja la mphamvu ya Mulungu.

70 Ndipo onse anati, Umo mtero, muli Mwana wa Mulungu kodi? Ndipo iye anati kwa iwo, 16 Munena kuti ndine.

71 Ndipo iwo anati, 17 Tifuniranjinso mboni? pakuti ife tokha tinamva m'kamwa mwa iye mwini.

23

1 Ndipo khamu lonselo Iinanyamuka kupita naye kwa Pilato.

2 Ndipo anayamba kumnenera iye, kuti, Tinapeza munthu uyu alikupandutsa anthu a mtundu wathu, ndi kuwaletsa kupereka msonkho kwa Kaisara, nadzinenera kuti iye yekha ndiye Kristu mfumu.

3 Ndipo Pilato anamfunsa iye, nanena, Kodindiwe mfumu ya Ayuda? Ndipo iye anamyankha nati, Mwatero.

4 Ndipo Pilato anati kwa ansembe akuru ndi makamu a anthu, Ndiribe kupeza cifukwa ca mlandu ndi munthu uyu.

5 Koma iwo anapunda kunena kuti, Amautsa anthuwo, naphunzitsa m'Yudeya lonse, kuyambira ku Galileya ndi kufikira kuno komwe.

6 Koma pamene Pilato anamva, anafunsa ngati munthuyu ali Mgalileya.

7 Ndipo m'mene anadziwa kuti ali wa m'ulamuliro wace wa Herode, anamtumiza iye kwa Herode, amene anali iye mwini ku Yerusalemu masiku awa,

8 Ndipo Herode, pamene anaona Yesu, anakondwa ndithu; pakuti anayamba kale kufuna kumpenya iye, cifukwa anamva za iye; nayembekeza kuona cizindikilo cina cocitidwa ndi iye.

9 Ndipo anamfunsa iye mau ambiri; koma iye sanamyankha kanthu.

10 Ndipo ansembe akuru ndi alembi anaimirira, namnenera iye kolimba.

11 Ndipo Herode ndi asilikari ace anampeputsa iye, namnyoza, nambveka iye copfunda conyezimira, nambwezera kwa Pilato.

12 Ndipo Herode ndi Pilato anaci-I tana cibwenzi tsiku lomwelo; pakuti kale anadana.

13 Ndipo Pilato anaitana ansembe akuru, ndi akuru, ndi anthu, asonkhane,

14 nati kwa iwo, Munadza kwa ine ndi munthu uyu ngati munthu wakupandutsa anthu: ndipo taonani, Ine ndinamfunsa za mlanduwu pamaso panu, ndipo sindinapeza pa munthuyu cifukwa ca zinthu zimene mumnenera;

15 inde, nga khale Herode yemwe; pakuti iye anambwezera iye kwa ife; ndipo taonani, sanacita iye kanthu kakuyenera kufa.

16 Cifukwacace ndidzamkwapula ndi kununasula iye. [

17 ]

18 Koma iwo onse pamodzi anapfuula, nati, Cotsani munthu uyu, mutimasulire Baraba;

19 ndiye munthu anaponyedwa m'ndende cifukwa ca mpanduko m'mudzi ndi ca kupha munthu.

20 Ndipo Pilato analankhulanso nao, nafuna kumasula Yesu;

21 koma iwo anapfuula, nanena, Mpacikeni, mpacikeni pamtanda.

22 Ndipo anati kwa iwo nthawi yacitatu, Nanga munthuyu anacita coipa ciani? Sindinapeza cifukwa ca kufera iye; cotero ndidzamkwapula iye ndi kummasula.

23 Koma anakakamiza ndi mau okweza, napempha kuti iye apacikidwe, Ndipo mau ao analakika.

24 Ndipo Pilato anaweruza kuti cimene alikufunsa cicitidwe.

25 Ndipo anawamasulira amene adaponyedwa m'ndende cifukwa ca mpanduko ndi kupha munthu, amene iwo anampempha; koma anapereka Yesu mwa cifuniro cao.

26 Ndipo popita naye, anagwira munthu, Simoni wa ku Kurene, alikucokera kuminda, namsenza iye mtanda aunyamule pambuyo pace pa Yesu,

27 Ndipo unamtsata unyinji waukuru wa anthu, ndi wa akazi amene anadziguguda pacifuwa, namlirira iye.

28 Koma Yesu anawapotolokera nati, Ana akazi inu a Yerusalemu, musandilirire Ine, koma mudzilirire nokha ndi ana anu.

29 Cifukwa taonani masiku alinkudza, pamene adzati, Odala ali ouma ndi mimba yosabala, ndi mawere osayamwitsa.

30 Pomwepo adzayamba kunena kwa mapiri, Igwani pa ife; ndi kwa zitunda, Bisani ife.

31 Pakuti ngati azicitira izi mtengo wauwisi, nanga kudzatani ndi wouma?

32 Ndipo analinso awiri ena, ndiwo ocita zoipa; anatengedwa pamodzi ndi iye kuti aphedwe.

33 Ndipo pamene anafika ku malo dzina lace Bade, anampacika iye pamtanda pomwepo, ndi ocita zoipa omwe, mmodzi ku dzanja lamanja ndi wina kulamanzere.

34 Ndipo Yesu ananena, Atate, muwakhululukire iwo, pakuti sadziwa cimene acita. Ndipo anagawana zobvala zace, poyesa maere.

35 Ndipo anthu anaima alikupenya, Ndi akurunso anamlalatira iye nanena, Anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati iye ndiye Kristu wa Mulungu, wosankhidwa wace.

36 Ndipo asilikarinso anamnyoza, nadza kwa iye, nampatsa vinyo wosasa,

37 nanena, Ngati Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda, udzipulumutse wekha.

38 Ndipo kunalinso lembo pamwamba pace, ndilo: UYU NDIYE MFUMU YAAYUDA.

39 Ndipo mmodzi wa ocita zoipa anapacikidwawo anamcitira iye mwano nanena, Kodi suli Kristu Iwe? udzipulumutse wekha ndi ife.

40 Koma winayo anayankha, namdzudzula iye, nati, Kodi suopa Mulungu, poona uli m'kulangika komweku?

41 Ndipo ifetu kuyenera; pakuti tirikulandira zoyenera zimene tinazicita: koma munthu uyu sanacita kanthu kolakwa.

42 Ndipo ananena, Yesu, ndikumbukileni m'mene mulowa Ufumuwanu.

43 Ndipo Iye ananena naye, Indetu, ndinena ndi iwe, Lero lino udzakhala ndine m'Paradaiso.

44 Ndipo ora lace pamenepo linali ngati lacisanu ndi cimodzi. Ndipo panali mdima pa dziko lonse kufikira ora lacisanu ndi cinai, ndipo dzuwa linada.

45 Ndipo nsaru yocinga ya m'Kacisi inang'ambika pakati.

46 Ndipo pamene Yesu anapfuula ndi mau akuru, anati, 1 Atate, m'manja mwanu ndipereka mzimu wanga. Ndipo pakutero anapereka mzimu wace.

47 Ndipo 2 pamene kenturiyo anaona cinacitikaco, analemekeza Mulungu, nanena, Zoonadi munthu uyu anali wolungama.

48 Ndipo makamu onse osonkhana kudzapenya ici, pamene anaona zinacitikazo, anapita kwao ndi kudziguguda pacifuwa.

49 Ndipo 3 omdziwa iye onse, ndi akazi amene adamtsata kucokera ku Galileya, anaima kutari, naona zinthu izi.

50 Ndipo taonani, munthu dzina lace Yosefe, ndiye mkuru wa mirandu, munthu wabwino ndi wolungama

51 (amene sanabvomereza kuweruza kwao ndi nchito yao) wa ku Arimateya, mudzi wa Ayuda, ndiye woyembekezera Ufumu wa Mulungu,

52 yemweyo anapita kwa Pilato napempha mtembo wace wa Yesu.

53 Ndipo 4 anautsitsa, naukulunga m'nsaru yabafuta, nauika m'manda osemedwa m'mwala, m'menemo sanaika munthu ndi kale lonse.

54 Ndipo panali tsiku lokonzera, ndi Sabata linayandikira.

55 Ndipo 5 akazi, amene anacokera naye ku Galileya, anatsata m'mbuyo, naona manda, ndi maikidwe a mtembo wace.

56 Ndipo anapita kwao, 6 nakonza zonunkhira ndi mafuta abwino. Ndipo pa Sabata anapumula 7 monga mwa lamulo.

24

1 Koma tsiku loyamba la sabata, mbanda kuca, anadza kumanda atatenga zonunkhira adazikonza.

2 Ndipo anapeza mwala unakunkhunizidwa kuucotsa pamanda.

3 Ndipo m'mene analowa sanapeza mtembo wa Ambuye Yesu.

4 Ndipo kunali, m'mene anathedwa nzeru naco, taonani amuna awiri anaimirira pafupi pao atabvala zonyezimira;

5 ndipo m'mene anakhala ndi mantha naweramira pansi nkhope zao, anati kwa iwo, Mufuniranji wamoyo pa akufa?

6 Palibe kuno iye, komatu anauka; kumbukilani muja adalankhula nanu, pamene analinso m'Galileya,

7 ndi kunena, kuti, Mwana wa munthu ayenera kuperekedwa m'manja a anthu ocimwa, ndi kupacikidwa pamtanda, ndi kuuka tsiku lacitatu.

8 Ndipo anakumbukila mau ace, nabwera kucokera kumanda,

9 nafotokozera zonse khumi ndi mmodziwo, ndi otsala onse omwe.

10 Koma panali Mariya wa Magadala, ndi Y ohana, ndi Mariya amace wa Yakobo, ndi akazi ena pamodzi nao amene ananena izi kwa atumwiwo.

11 Ndipo mau awa anaoneka pamaso pao ngati nkhani zacabe, ndipo sanamvera akaziwo.

12 Koma Petro ananyamuka nathamangira kumanda, ndipo powerama anaona nsaru zoyera pa zokha; ndipo anacoka nanka kwao, nazizwa ndi cija cidacitikaco.

13 Ndipo taonani, awiri a mwa iwo analikupita tsiku lomwelo kumudzi dzina lace Emau, wosiyana ndi Yerusalemu mastadiya makumi asanu ndi limodzi.

14 Ndipo iwowa anakambirana nkhani za izi zonse zidacitika.

15 Ndipo kunali m'kukambirana kwao ndi kufunsana, Yesu mwini anayandikira, natsagana nao.

16 Koma maso ao anagwidwa kuti asamzindikire iye.

17 Ndipo anati kwa iwo, Mau awa ndi otani mulandizanawo poyendayenda? Ndipo anaima ndi nkhope zao zacisoni.

18 Ndipo mmodzi wa iwo, dzina lace Kleopa, anayankha nati kwa iye, Kodi iwe wekha ndiwe mlendo m'Yerusalemu ndi wosazindikira zidacitikazi masiku omwe ano?

19 Ndipo anati kwa iwo, Zinthu zanji? Ndipo anati kwa iye, lzi za Yesu Mnazarene, ndiye munthu mneneri wamphamvu m'nchito, ndi m'mau, pamaso pa Mulungu ndi anthu onse;

20 ndikuti ansembe akulu ndi akulu athu anampereka iye ku ciweruziro ca imfa, nampacika iye pamtanda.

21 Ndipo tinayembekeza ife kuti iye ndiye wakudzayo kudzaombola Israyeli, Komatunso, pamodzi ndi izi zonse lero ndilo tsiku lacitatu kuyambira zidacitika izi.

22 Komatu akazi enanso a mwa ife anatidabwitsa, ndiwo amene analawirira kumanda;

23 ndipo m'mene sanapeza mtembo wace, anadza, nanena kuti adaona m'masomphenya angelo, amene ananena kuti ali ndi moyo iye.

24 Ndipo ena a iwo anali nafe anacoka kunka kumanda, napeza monga momwe akazi adanena; koma Iyeyo sanamuona.

25 Ndipo iye anati kwa iwo, Opusa inu, ndiozengereza mtima kusakhulupirira zonse adazilankhula aneneri!

26 Kodi sanayenera Kristu kumva zowawa izi, ndi kulowa ulemerero wace?

27 Ndipo anayamba kwa Mose, ndi kwa aneneri onse, nawatanthauzira iwo m'malembo onse zinthu za iye yekha.

28 Ndipo anayandikira ku mudzi umene analikupitako; ndipo anacita ngati anafuna kupitirira.

29 Ndipo anamuumiriza iye, nati, Khalani ndi ife; pakuti kuli madzulo, ndipo dzuwa lapendekatu, Ndipo analowa kukhala nao.

30 Ndipo kunali m'mene iye anaseama nao pacakudya, anatenga mkate, naudalitsa naunyema, napatsa iwo.

31 Ndipo maso ao anatseguka, ndipo anamzindikira iye; ndipo anawakanganukira iye, nawacokera.

32 Ndipo anati wina kwa mnzace, Mtima wathu sunali wotentha m'kati mwathu nanga m'mene analankhula nafe m'njira, m'mene anatitseguliramalembo?

33 Ndipo ananyamuka nthawi yomweyo nabwera ku Yerusalemu, napeza khumi ndi mmodziwo, ndi iwo anali nao atasonkhana pamodzi,

34 nanena, Ambuye anauka ndithu, naonekera kwa Simoni.

35 Ndipo iwo anawafotokozera za m'njira, ndi umo anadziwika nao m'kunyema kwa mkate.

36 Ndipo pakulankhula izi iwowa, iye anaimirira pakati pao; nanena nao, Mtendere ukhale nanu.

37 Koma anaopsedwandi kucita mantha, 1 nayesa alikuona mzimu.

38 Ndipo anati kwa iwo, Mukhala bwanji obvutika? ndipo matsutsano am auka bwanji m'mtima mwanu?

39 Penyani manja anga ndi mapazianga, kuti Ine ndine mwini: 2 ndikhudzeni, ndipo penyani; pakuti mzimu ulibe, mnofu ndi mafupa, monga muona ndirinazo Ine.

40 Ndipo m'mene ananena ici, anawaonetsera iwo manja ace ndi mapazi ace.

41 Koma pokhala iwo cikhalire osakhulupirira cifukwa ca cimwemwe, nalikuzizwa, anati kwa iwo, 3 Muli nako kanthu kakudya kuno?

42 Ndipo anampatsa iye cidutsu ca nsomba yokazinga.

43 Ndipo 4 anacitenga, nacidya pamaso pao.

44 Ndipo anati kwa iwo, 5 Awa ndi mauwo ndinalankhula nanu, paja ndinakhala ndi inu, kuti ziyenera kukwanitsidwa zonse zolembedwa za Ine m'cilamulo ca 6 Mose, ndi aneneri, ndi masalmo.

45 Ndipo 7 anawatsegulira mitima yao, kuti adziwitse malembo;

46 ndipo anati kwa iwo, 8 Kotero kwalembedwa, kuti Kristu amve zowawa, nauke kwa akufa tsiku lacitatu;

47 ndi kuti kulalikidwe m'dzina lace kulapa ndi 9 kukhululukidwa kwa macimo kwa 10 mitundu yonse, kuyambira ku Yerusalemu.

48 11 Inu ndinu mboni za izi.

49 Ndipo onani, 12 Ine nditumiza pa inu lonjezano la Atate wanga; koma khalani inu m'mudzi muno, kufikira mwabvekedwa ndi mphamvu yocokera Kumwamba.

50 Ndipo anaturuka nao kufikira ku Betaniya; nakweza manja ace, nawadalitsa.

51 Ndipo kunali, 13 pakuwadalitsa iye analekana nao, natengedwa kunka Kumwamba.

52 Ndipo 14 anamlambira iye, nabwera ku Yerusalemu ndi cimwemwe cacikuru;

53 ndipo IS anakhala ci khalire m'Kacisi, nalikuyamika Mulungu, Amen.