1 NDIPO masiku akuweruza oweruzawo munali njala m'dziko. Ndipo munthu wa ku Betelehemu-Yuda anamuka nakagonera m'dziko la Moabu, iyeyu, ndi mkazi wace, ndi ana ace amuna awiri.
2 Dzina la munthuyo ndiye Elimeleki, ndi dzina la mkazi wace ndiye Naomi, ndi maina a ana ace awiri ndiwo Maloni, ndi Kilioni; ndiwo a ku Efrata ku Betelelehemu-Yuda. Iwowa ndipo analowa m'dziko la Moabu, nakhala komweko.
3 Ndipo Elimeleki mwamuna wace wa Naomi anamwalira; natsala iye ndi ana ace awiri.
4 Nadzitengera iwo akazi a ku Moabu; wina dzina lace ndiye Olipa, mnzace dzina lace ndiye Rute; ndipo anagonera komweko ngati zaka khumi.
5 Koma Maloni ndi Kilioni anamwalira onse awiri; motero ana ace amuna awiri ndi mwamuna wace anamsiya mkaziyo.
6 Pamenepo ananyamuka iyeyu ndi apongozi ace kuti abwerere kucoka m'dziko la Moabu; pakuti adamva m'dziko la Moabu kuti Yehova adasamalira anthu ace ndi kuwapatsa cakudya.
7 Naturuka iye kumene anakhalako ndi apongozi ace awiri pamodzi naye; namka ulendo wao kubwererakudzikola Yuda.
8 Ndipo Naomi anati kwa apongozi ace awiri, Mukani, bwererani yense wa inu ku nyumba ya amai wace; Yehova akucitireni zokoma, monga umo munacitira akufa aja ndi ine.
9 Yehova akuloleni mupeze mpumulo yense m'nyumba ya mwamuna wace. Nawapsompsona, nakweza iwo mau ao nalira misozi.
10 Ndipo ananena naye, Iai, koma tidzapita nanu kwa anthu a kwanu.
11 Nati Naomi, Bwererani, ana anga, mudzatsagana nane bwanji? ngati ndiri nao m'mimba mwanga ana amuna ena kuti akhale amuna anu?
12 Bwererani, ana anga, mukani, pakuti ndakalambitsa ine, sindikhoza kukhala naye mwamuna. Ngakhale ndikati, Ndiri naco ciyembekezo, ndikakhala naye mwamuna usiku uno, ndi kubalanso ana amuna;
13 kodi mudzawalindirira akakula? mudzadziletsa osakwatibwa? Iai, ana anga, pakuti candiwawa koposa cifukwa ca inu popeza dzanja la Yehova landiturukira.
14 Nakweza iwo mau ao, naliranso misozi; ndi Olipa anampsompsona mpongozi wace, koma Rute anamkangamira.
15 Pamenepo anati, Taona mbale wako wabwerera kwa anthu a kwao, ndi kwa mulungu wace, bwerera umtsate mbale wako.
16 Nati Rute, Musandiumirize kuti ndikusiyeni, ndi kubwerera osakutsatani; pakuti kumene mumukako ndimuka inenso, ndi kumene mugonako ndigona inenso; anthu a kwanu ndiwo anthu a kwa inenso, ndi Mulungu wanu ndiye Mulungu wanga;
17 kumene mudzafera inu ine ndidzafera komweko, ndi kuikidwa komweko; andilange Yehova naonjezeko, ciri conse cikasiyanitsa inu ndi ine, koma imfa ndiyo.
18 Ndipo pakuona kuti analimbika kumuka naye, analeka kulankhula naye.
19 Namuka iwo awiriwo mpaka anafika ku Betelehemu. Ndipo kunali pakufika iwo ku Betelehemu, mudzi wonse unapokosera za iwo; nati, Kodi uyu ndi Naomi?
20 Koma ananena nao, Musandicha Naomi, mundiehe Mara; pakuti Wamphamvuyonse anandicitira zowawa ndithu.
21 Ndinacoka pane wolemera, nandibwezanso kwathu Yehova wopanda kanthu; mundicheranji Naomi, popeza Yehova wandicitira umboni wakunditsutsa, ndi Wamphamvuyonse wandicitira cowawa?
22 Momwemo anabwera Naomi ndi Rute Mmoabu mpongozi wace pamodzi naye, amene anabwera kucokera ku dziko la Moabu; ndipo anafika ku Betelehemu, pakuyamba anthu kuceka barele.
1 Ndipo Naomi anali nave mbale wa mwamuna wace, ndiye munthu mwini cuma cambiri wa banja la Elimeleki; dzina lace ndiye Boazi.
2 Nati Rute Mmoabu kwa Naomi, Mundilole ndimuke kumunda, ndikatole khunkha is ngala za tirigu, kumtsata iye amene adzandikomeramtima. Nanena naye, Muka, mwana wanga.
3 Namuka iye, nakatola khunkha m'munda namatsata ocekawo; ndipo kudangotero naye kuti deralo la munda linali la Boazi, ndiye wa banja la Elimeleki.
4 Ndipo taona, Boazi anafuma ku Betelehemu, nati kwa oceka, Yehova akhale nanu. Namyankha iwo, Yehova akudalitseni.
5 Nati Boazi kwa mnyamata wace woyang'anira ocekawo, Mkazi uyu ngwa yani?
6 Ndipo mnyamata woyang'anira ocekawo anayankha nati, Ndiye mkazi Mmoabuyo anabwera ndi Naomi ku dziko la Moabu;
7 ndipo anati, Undilole, ndikunkhe ndiole pakati pa mitolo potsata ocekawo; nadza iye nakhalakhala kuyambira m'mawa mpaka tsopano; koma m'nyumba samakhalitsamo.
8 Pamenepo Boazi ananena ndi Rute, Ulikumva, mwana wanga? Usakakunkha m'munda mwina, kapena kupitirira pano, koma uumirire adzakazi anga mommuno.
9 Maso ako akhale pa munda acekawo, ndi kuwatsata; kodi sindinawauza anyamata asakukhudze? Ndipo ukamva ludzu, muka kumitsuko, ukamweko otunga anyamatawo,
10 Potero anagwa nkhope yace pansi, nadziweramira pansi, nanena naye, Mwandikomera mtima cifukwa ninji kuti mundisamalira ine, popeza ndine mlendo?
11 Ndipo Boazi anayankha nanena naye, Anandifotokozera bwino zonse unacitira mpongozi wako atafa mwamuna wako; ndi kuti wasiya atate wako ndi mako, ndi dziko lobadwirako iwe, ndi kudza kwa anthu osawadziwa iwe kale.
12 Yehova akubwezere nchito yako, nakupatse mphotho yokwanira Yehova, Mulungu wa Israyeli, amene unadza kuthawira pansi pa mapiko ace.
13 Nati iye, Mundikomere mtima mbuye wanga, popeza mwandisangalatsa, popezanso mwanena cokondweretsa mtima wa mdzakazi wanu, ndingakhale ine sindine ngati mmodzi wa adzakazi anu.
14 Ndipo pa nthawi ya kudya Boazi ananena naye, Sendera kuno, nudyeko mkate; nusunse nthongo yako m'vinyo wosasayo. Nakhala iye m'mbali mwa ocekawo; ndipo anamtambasulira dzanja kumninkha tirigu wokazinga, nadya iye, nakhuta, nasiyapo.
15 Ndipo ataumirira kukatola khunkha, Boazi analamulira anyamata ace ndi kuti, Atole khunkha ngakhale pakati pa mitolo, musamcititse manyazi.
16 Ndiponso mumtayire za m'manja, ndi kuzisiya, natole khunkha, osamdzudzula.
17 Natola khunka iye m'munda mpaka madzulo; naomba khunkhalo napeza ngati licero la barele,
18 nalisenza nalowa kumudzi; ndipo mpongozi wace anaona khunkhalo; Rute naturutsanso nampatsa mkute uja anausiya atakhuta.
19 Ndipo mpongozi wace ananena naye, Unakatola kuti khunkha lero? ndi nchito udaigwira kuti? Adalitsike iye amene anakusamalira. Ndipo anamfotokozera mpongozi wace munthu amene anakagwirako nchito, nati, Dzina lace la munthuyo ndinakagwirako nchito lero ndiye Boazi.
20 Nati Naomi kwa mpongozi wace, Yehova amdalitse amene sanaleka kuwacitira zokoma amoyo, ndi akufa. Ndipo Naomi ananena baye, Munthuyu ndiye mbale wathu, ndiye mmodzi wa iwo otiombolera colowa.
21 Ndipo Rute Mmoabu anati, Ananenanso nane ndithu, Uwaumirire anyamata anga, mpaka atatha kuceka zanga zonse za m'minda.
22 Nati Naomi kwa Rute mpongozi wace, Ncabwino, mwana wanga, kuti uzituruka nao adzakazi ace, ndi kuti asakukomane m'munda wina uti wonse.
23 Momwemo anaumirira adzakazi a Boazi kuti atole khunkha kufikira atatha kuceka barele ndi tirigu; ndipo anakhala iye kwao kwa mpongozi wace.
1 Pamenepo Naomi mpongozi wace ananena naye, Mwana wanga, kodi ndisakufunire popumulako, kuti ukhale bwino?
2 Nanga Boazi wodziwana nafe, amene unakhala nao adzakazi ace? Taona, usiku uno apuntha barele popunthirapo.
3 Usambe tsono, nudzole, nubvale zobvala zako, nutsikire popunthirapo, koma usadziwike naye munthuyo, koma atatha kudya ndi kumwa ndiko.
4 Ndipo kudzali, akagona, upenye apo ati agone, numuke, nubvundukule ku mapazi ace, nugone, ndi iyeyo adzakufotokozera zoyenera kucita iwe.
5 Ndipo ananena naye, Zonse muzinena ndidzacita.
6 Pamenepo anatsikira popunthirapo, nacita zonse monga umo mpongozi wace adamuuza.
7 Ndipo atatha Boazi kudya ndi kumwa, nusekerera mtima wace, anakagona kuthungo kwa mulu wa tirigu; nadza iye kacetecete, nabvuodukula ku mapazi ace, nagona.
8 Ndipo kunali, pakati pa usiku munthuyo anadzidzimuka, natembenuka; ndipo taona pa mapazi ace pagona mkazi.
9 Nati iye, Ndiwe yani? Nayankha iye, Ndine Rute mdzakazi wanu; mupfunde mdzakazi wanu copfunda canu, pakuti inu ndinu wondiombolera colowa.
10 Nati iye, Yehova akudalitse, mwana wanga. Cokoma cako wacicita potsiriza pano, ciposa cakuyamba cija, popeza sunatsata anyamata, angakhale osauka angakhale acuma.
11 Ndipo tsopano, mwana wanga, usaope; ndidzakucitira zonse unenazi; pakuti onse a pa mudzi wa anthu a mtundu wanga adziwa kuti iwe ndiwe mkazi waulemu.
12 Tsopano ndipo, zoonadi, ine ndine wakukuombolera colowa, koma pali wakukuombolera woposa ine.
13 Gona usiku uno, ndipo kudzali m'mawa, akakuombolera, cabwino, akuombolere; koma ngati safuna kukuombolera, pali Yehova, ndidzakuombolera colowa ndine; gona mpaka m'mawa.
14 Nagona ku mapazi ace mpaka m'mawa; nalawira asanazindikirane anthu, Pakuti anati, Cisadziwike kuti mkaziyo anadza popunthirapo,
15 Ndipo anati, Bwera naco copfunda cako, nucigwire; nacigwira iye; ndipo anayesa miyeso isanu ndi umodzi ya barele, namsenza; atatero analowa m'mudzi.
16 Ndipo pamene anadza kwa mpongozi wace, iye anati, Wapeza bwanji, mwana wanga? Pamenepo anamfotokozera zonse anamcitira munthuyo.
17 Natinso, Miyeso iyi isanu ndi umodzi ya barele anandipatsa, pakuti anati, Usafike kwa mpongozi wako wopanda kanthu.
18 Ndipo anati, Khala ulipo, mwana wanga; mpaka udziwa umo ukhalire mlandu; pakuti munthuyo sadzauleka mpaka atautha mlanduwo lero lino.
1 Ndipo Boazi anakwera kumka kucipata, nakhala pansi pomwepo; ndipo taona, woombolera winayo adanena Boazi analinkupita; nati iye, Iwe uje, pambuka, khala pansi apa; napambuka iye, nakhala pansi.
2 Ndipo anatenga amuna khumi a akulu a mudzi, nati, Mukhale pansi apa. Nakhala pansi iwo.
3 Pamenepo anati kwa woombolerayo, Naomi anabwerayo ku dziko la Moabu ati agulitse kadziko kala kadali ka mbale wathu Elimeleki;
4 ndipo ndati ndikuululira ici, ndi kuti, Ugule aka pamaso pa nzika, ndi pamaso pa akulu a anthu a kwathu. Ukafuna kuombola ombola; koma ukapanda kuombola, undiuze, ndidziwe; pakuti palibe woombola koma iwe, ndi ine pambuyo pako. Pamenepo anati, Ndidzaombola.
5 Nati Boazi, Tsiku lomwelo ugula mundawo pa dzanja la Naomi, uugulanso kwa Rute, Mmoabu, mkazi wa wakufayo, kuukitsira dzina la wakufayo pa colowa cace.
6 Ndipo woombolerayo anati, Sindikhoza kuuombola kwa ine ndekha, ndingaononge colowa canga; udzitengere wekha mphamvu yanga yakuombola; popeza sinditha kuombola.
7 Koma kale m'Israyeli pakuombola ndi pakusinthana, kutsimikiza mlandu wonse, akatero: munthu abvula nsapato yace, naipereka kwa mnansi wace; ndiwo matsimikizidwe m'Israyeli.
8 Ndipo woombolayo anati kwa Boazi, Udzigulire wekha kadzikoko. Nabvula nsapato yace.
9 Nati Boazi kwa akulu, ndi kwa anthu onse, Inu ndinu mboni lero lino kuti ndagula zonse za Elimeleki, ndi zonse za Kilioni, ndi Maloni, pa dzanja la Naomi.
10 Ndiponso Rute Mmoabu, mkazi wa Maloni ndamgula akhale mkazi wanga kuukitsa dzina la wakufayo pa colowa cace; kuti dzina la wakufayo lisaiwalike pakati pa abale ace, ndi pa cipata ca malo ace; inu ndinu mboni lero lino.
11 Pamenepo anthu onse anali kucipata, ndi akuru, anati, Tiri mboni ife. Yehova acite kuti mkazi wakulowayo m'nyumba mwako ange Rakele ndi Leya, amene anamanga nyumba ya Israyeli, iwo awiri; nucite iwe moyenera m'Efrata, numveke m'Betelehemu;
12 ndi nyumba yako inge nyumba ya Perezi, amene Tamare anambalira Yuda, ndi mbeu imene Yehova adzakupatsa ya namwali uyu.
13 Momwemo Boazi anatenga Rute, nakhala iye mkazi wace; ndipo analowa kwa iye; nalola Yehova kuti aime, ndipo anabala mwana wamwamuna.
14 Pamenepo akazi anati kwa Naomi, Adalitsike Yehova amene sana lola kuti akusowe woombolera lero; nilimveke dzina lace m'Israyeli,
15 Nakhale uyu wakukubwezera moyo, ndi wodyetsa ukalamba wako; pakuti mpongozi wako amene akukonda, amene aposa ana amuna asanu ndi awiri kukuthandiza, anambala.
16 Ndipo Naomi anamtenga mwanayo, namuika pacifuwa pace, nakhala mlezi wace.
17 Ndi akazi anansi ace anamucha dzina, ndi kuti, Kwa Naomi kwambadwira mwana; namucha dzina lace Ohedi; ndiye atate wa Jese atate wa Davide.
18 Iyo ndiyo mibadwo ya Perezi; Perezi anabala Hezironi;
19 ndi Hezironi anabala Ramu, ndi Ramu anabala Aminadabu;
20 ndi Aminadabu anabala Nasoni, ndi Nasoni anabala Salimoni;
21 ndi Salimoni anabala Boazi, ndi Boazi anabala Obedi;
22 ndi Obedi anabala Jese, ndi Jese anabala Davide.