1 SIMONI Petro, kapolo ndi mtumwi wa Yesu Kristu kwa iwo amene adalandira cikhulupiriro ca mtengo wace womwewo ndi ife, m'cilungamo ca Mulungu wathu ndi Mpulumutsi Yesu Kristu:
2 Cisomo kwa inu ndi mtendere zicurukitsidwe m'cidziwitso ca Mulungu ndi Yesu Ambuye wathu.
3 Popeza mphamvu ya umulungu wace idatipatsa ife zonse za pamoyo ndi cipembedzo, mwa cidziwitso ca iye amene adatiitana ife ndi ulemerero ndi ukoma wace wa iye yekha;
4 mwa izi adatipatsa malonjezano a mtengo wace ndi akuru ndithu; kuti mwa izi mukakhale oyanjana nao umulungu wace, mutapulumuka ku cibvundi ciri pa dziko lapansi m'cilakolako.
5 Ndipo mwa ici comwe, pakutengeraponso cangu conse, muonjezerapo ukoma pa cikhulupiriro canu, ndi paukoma cizindikiritso; ndi pacizindikiritso codziletsa;
6 ndi pacodziletsa cipiriro;
7 ndi pacipiriro zipembedzo; ndi pactpembedzo cikondi ca pa abale; ndi pacikondi ca pa abale cikondi.
8 Pakuti izi zikakhala ndi inu, ndipo zikacuruka, zidzacita kuti musakhale aulesi kapena opanda zipatso pa cizindikiritso ca Ambuye wathu Yesu Kristu.
9 Pakuti iye wakusowa izi ali wakhungu, wa cimbuuzi, woiwala matsukidwe ace potaya zoipa zace zakale,
10 Momwemo abale, onjezani kucita cangu kukhazikitsa maitanidwe ndi masankhulidwe anu; pakuti mukacita izi, simudzakhumudwa nthawi zonse;
11 pakuti kotero kudzaonjezedwa kwa inu kolemerera khomo lakulowa ufumu wosatha wa Ambuye wathu ndi Mpulumutsi Yesu Kristu.
12 Mwa ici sindidzaleka kukukumbutsani inu nthawi zonse za izi, mungakhale muzidziwa nimukhazikika m'coonadi ciri ndi inu.
13 Ndipo ndiciyesa cokoma, pokhala ine m'msasa uwu, kukutsitsimutsani ndi kukukumbutsani;
14 podziwa kuti kuleka kwa msasa wanga kuli pafupi, monganso Ambuye wathu Yesu Kristu anandilangiza.
15 Koma ndidzacitanso cangu kosalekeza kuti nditacoka ine, mudzakhoza kukumbukila izi,
16 Pakuti sitinatsata miyambi yacabe, pamene tinakudziwitsani mphamvu ndi maonekedwe a Ambuye wathu Yesu Kristu, koma tinapenya m'maso ukulu wace.
17 Pakuti analandira kwa Mulungu Atate ulemu ndi ulemerero, pakumdzera iye mao otere ocokera ku ulemerero waukuru, Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa, amene Ine ndikondwera naye;
18 ndipo mau awa ocokera Kumwamba tidawamva ife, pokhala pamodzi ndi iye m'phiri lopatulika lija,
19 Ndipo tiri nao mau a cinenero okhazikika koposa; amene mucita bwino powasamalira, monga nyali younikira m'malo a mdima, kufikira kukaca, nikauka nthanda pa mtima yanu;
20 ndi kudziwa ici poyamba, kuti palibe cinenero ca lembo citanthauzidwa pa cokha,
21 pakuti kale lonse cinenero sicinadza ndi cifuniro ca munthu; koma anthu a Mulungu, ogwidwa ndi Mzimu Woyera, analankhula.
1 Koma padakhalanso pakati pa anthuwo aneneri onama, monganso padzakhala aphunzitsi onama pakati pa inu, amene adzalowa nayo m'tseri mipatuko yotayikitsa, nadzakana Ambuye amene adawagula, nadzadzitengera iwo okha citayiko cakudza msanga.
2 Ndipo ambiri adzatsata zonyansa zao; cifukwa ca iwo njira ya coonadi idzanenedwa zamwano.
3 Ndipo m'cisiriro adzakuyesani malonda ndi mau onyenga; amene ciweruzo cao sicinacedwa ndi kale lomwe, ndipo citayiko cao siciodzera.
4 Pakuti ngati Mulungu sanalekerera angelo adacimwawo, koma anawaponya kundende nawaika ku maenje a mdima, asungike akaweruzidwe;
5 ndipo sanalekerera dziko lapansi lakale, koma anasunga Nowa mlaliki wa cilungamo, ndi anzace asanu ndi awiri, pakulitengera dziko la osapembedza cigumula;
6 ndipo pakuisandutsa makara midzi ya Sodoma ndi Gomora anaitsutsa poigwetsa, ataiika citsanzo ca kwa iwo akakhala osapembedza;
7 ndipo anapulumutsa Loti wolungamayo, wolema mtima ndi mayendedwe onyansa a oipa aja
8 (Pakuti wolungamayo pokhala pakati pao, ndi kuona ndi kumva zao, anadzizunzira moyo wace wolungama tsiku ndi tsiku ndi nchito zao zosayeruzika).
9 Ambuye adziwa kupulumutsa opembedza poyesedwa iwo, ndi kusunga osalungama kufikira tsiku loweruza akalangidwe;
10 kama makamaka iwo akutsata zathupi, m'cilakolako ca zodetsa, napeputsa cilamuliro; osaopa kanthu, otsata cifuniro ca iwo eni, santhunthumira kucitira mwano akulu;
11 popeza angelo, angakhale awaposa polimbitsa mphamvu, sawaneneza kwa Ambuye mlandu wakucita mwano.
12 Koma awo, ngati zamoyo zopanda nzeru, nyama zobadwa kuti zikodwe ndi kuonongedwa, akucitira mwano pa zinthu osazidziwa, adzaonongeka m'kuononga kwao,
13 ocitidwa zoipa kulipira kwa cosalungama; anthu akuyesera cowakondweretsa kudyerera usana; ndiwo mawanga ndi zirema, akudyerera m'madyerero acikondi ao, pamene akudya nanu;
14 okhala nao maso odzala ndi cigololo, osakhoza kuleka ucimo, kunyengerera iwo a moyo wosakhazikika; okhala nao mtima wozolowera kusirira; ana a temberero;
15 posiya njira yolunjika, anasokera, atatsata njira ya Balamu mwana wa Beori, amene anakonda mphotho ya cosalungama;
16 koma anadzudzulidwa pa kulakwa kwace mwini; buru wopanda mau, wolankhula ndi mau a munthu, analetsa kuyarukakwa mneneriyo.
17 Iwo ndiwo akasupe opanda madzi, nkhungu yokankhika ndi mkuntho; amene iadima wakuda bii uwasungikira,
18 Pakuti polankhula mau otukumuka opanda pace, anyengerera pa zilakolako za thupi, ndi zonyansa, iwo amene adayamba kupulumukira a mayendedwe olakwawo;
19 ndi kuwalonjezera iwo ufulu, pokhala iwo okha ali aka polo a cibvundi; pakuti iye amene munthu agonjedwa naye, ameneyonso adzakhala kapolo wace.
20 Pakuti ngati, adatha kuthawa zodetsa za dziko lapansi mwa cizindikiritsoca, Ambuye ndi Mpulumutsi Yesu Kristu, akodwanso nazo, nagonjetsedwa, zorsiriza zao zidzaipa koposa zoyambazo,
21 Pakuti pakadakhala bwino kwa iwo akadakhala osazindikira njira ya cilungamo, ndi poizindikira, kubwerera kutaya lamulo lopatulika lopatsidwa kwa iwo.
22 Cidawayenera iwo ca nthanthi yoona, Garu wabwerera ku masanzi ace, ndi nkhumba idasambayi yabwerera kukunkhulira m'thope.
1 Okondedwa, uyu ndiye kalata waciwiri ndilembera kwa inu tsopano; mwa onse awiri nditsitsimutsa mtima wanu woona ndi kukukumbutsani;
2 kuti mukumbukile mau onenedwa kale ndi aneneri oyera, ndi lamulo la Ambuye ndi Mpulumutsi, mwa atumwi anu;
3 ndi kuyamba kucizindikira ici kuti masiku otsiriza adzafika onyoza ndi kucita zonyoza, oyenda monga mwa zilakolako za iwo eni,
4 ndi kunena, Liri kuti lonjezano la kudza kwace? pakuti kuyambira kuja makolo adamwalira zonse zikhala monga ciyambire cilengedwe.
5 Pakuti ici aiwala dala, kuti miyamba inakhala kale lomwe, ndi dziko lidaungika ndi madzi ndi mwa madzi, pa mau a Mulungu;
6 mwa izi dziko lapansi la masiku aja, pomizika ndi madzi, lidaonongeka;
7 koma miyamba ndi dziko lamasiku ano, ndi mau omwewo zaikika kumoto, zosungika kufikira tsiku la ciweruzo ndi cionongeko ca anthu osapembedza.
8 Koma ici cimodzi musaiwale, okondedwa inu, kuti tsiku limodzi likhala kwa Ambuye ngati zaka cikwi, ndi zaka cikwi ngati tsiku limodzi.
9 Ambuye sazengereza nalo lonjezano, monga ena aciyesa cizengerezo; komatu aleza mtima kwa inu, wosafuna kuti ena aonongeke, koma kuti onse afike kukulapa.
10 Koma tsiku la Ambuye lidzadza ngati mbala; m'mene miyamba idzapita ndi cibumo cacikuru, ndi zam'mwamba zidzakanganuka ndi kurentha kwakukuru, ndipo dziko ndi nchito ziri momwemo zidzarenthedwa.
11 Popezaizi zonse zidzakanganuka kotero, muyenera inu kukhala anthu otani nanga, m'mayendedwe opatulika ndi m'cipembedzo,
12 akuyembekezera ndi kufulumira kwa kudza kwace kwa tsiku la Mulungu, m'menemo miyamba potentha mota idzakanganuka, ndi zam'mwamba zidzasungunuka ndi kutentha kwakukuru.
13 Koma monga mwa lonjezano lace tiyembekezera miyamba yatsopano, ndi ziko latsopano m'menemo mukhalitsa cilungamo.
14 Momwemo, okondedwa, popeza muyembekeza izi, citani cangu kuti mupezedwe ndi iye mumtendere, opanda banga ndi opanda cirema.
15 Ndipo yesani kulekerera kwa Ambuye wathu cipulumutso; monganso mbale wathu wokondedwa Paulo, monga mwa nzeru zopatsidwa cwa iye, anakulemberani;
16 monganso m'akalata ace onse pokanba momwemo za izi; m'menemo nuli zina zobvuta kuzizindikira, zinene anthu osaphunzira ndi osachazikika apotoza, monganso atero lao malembo ena, ndi kudziononga lao eni.
17 Inu, tsono, okondedwa, oozizindikiratu izi, cenjerani, kuti ootengedwa ndi kulakwa kwa iwo osayeruzika, mungagwe kusiya cichazikiko canu.
18 Koma kulani n'cisomo ndi cizindikiritso ca Ambure wathu ndi Mpulumutsi Yesu vistu; kwa iye kukhale uleme'ero, tsopano ndi nthawi zonse. Amen.