1

1 PETRO, mtumwi wa Yesu Kristu, kwa osankhidwa akukhala: alendo a cibalaliko a ku Ponto, Galatiya, Kapadokiya, Asiya, ndi Bituniya,

2 monga mwa kudziwiratu kwa Mulungu Atate, m'ciyeretso ca Mzimu, cocitira cimvero, ndi kuwaza kwa mwazi wa Yesu Kristu: Cisomo, ndi mtendere zicurukire inu.

3 Wodalitsika Mulungu ndiye Atate wa Ambuye wathu Yesu Kristu, iye amene, monga mwa cifundo cace cacikuru, anatibalanso ku ciyembekezo ca moyo, mwa kuuka kwa akufa kwa Yesu Kristu;

4 kuti tilandire colowa cosabvunda ndi cosadetsa ndi cosafota, cosungikira m'Mwamba inu,

5 amene musungidwa ndi mphamvu ya Mulungu mwa cikhulupiriro, kufikira cipulumutso cokonzeka kukabvumbulutsidwa nthawi yotsiriza.

6 M'menemo mukondwera, kungakhale tsopano kanthawi, ngati kuyenera, mukacitidwe cisoni ndi mayesero a mitundu mitundu,

7 kuti mayesedwe a cikhulupiriro canu, ndiwo a mtengo wace woposa wa golidi amene angotayika, ngakhale ayesedwa ndi moto, akapezedwe ocitira ciyamiko ndi ulemerero ndi ulemu pa bvumbulutso la Yesu, Kristu;

8 amene mungakhale simunamuona mumkonda; amene mungakhale simumpenya tsopano, pokhulupirira, mukondwera naye ndi, cimwemwe cosaneneka, ndi ca ulemerero:

9 ndi kulandira citsiriziro ca cikhulupiriro canu, ndico cipulumutso ca moyo wanu.

10 Kunena za cipulumutso ici anafunafuna nasanthula aneneri, pakunenera za cisomo cikudzerani;

11 ndi kusanthula nthawi yiti, kapena nthawi yanji Mzimu wa Kristu wokhala mwa iwo analozera, pakucitiratu umboni wa masautso a Kristu, ndi ulemerero, worsarana nao.

12 Kwa iwo amene kudabvumbulutsidwa, kuti sanadzitumikira iwo okha, koma inu, ndi zinthu izi, zimene zauzidwa kwa inu tsopano, mwa iwo amene anakulalikirani Uthenga Wabwino mwa Mzimu Woyera, wotumidwa kucokera Kumwamba; zinthu izi angelo alakalaka kusuzumiramo.

13 Mwa ici, podzimanga m'cuuno, kunena za mtima wanu, mukhale odzisunga, nimuyembekeze konse konse cisomo cirikutengedwa kudza naco kwa inu m'bvumbulutso la Yesu Kristu;

14 monga ana omvera osadzifanizitsanso ndi zilakolako zakale, pokhala osadziwa inu;

15 komatu monga iye wakuitana inu ali woyera mtima, khaiani inunso oyera mtima m'makhalidwe anu onse;

16 popeza kwalembedwa, Muzikhala oyera mtima, pakuti Ine ndine woyera mtima.

17 Ndipo mukamuitana ngati Alate, iye amene aweruza monga mwa nchito ya yense, wopanda tsankhu, khalani ndi mantha nthawi ya cilendo canu;

18 podziwa kuti simunaomboledwa ndi zobvunda, golidi ndi siliva, kusiyana nao makhalidwe anu acabe ocokera kwa makolo anu:

19 koma 1 ndi mwazi wa mtengo wace wapatali 2 monga wa mwana wa nkhosa wopanda cirema, ndi wopanda banga, ndiwo mwazi wa Kristu:

20 3 amene anazindikirikatu lisanakhazikike dziko lapansi, koma anaonetsedwa pa citsiriziro ca nthawi,

21 cifukwa ca inu amene mwa rye mukhulupirira Mulungu 4 wakwnuukitsa iye kwa akufa, ndi kumpatsa iye ulemerero; kotero kuti cikhulupiriro canu ndi ciyembekezo canu cikhale pa Mulungu.

22 Popeza 5 mwayeretsa moyo wanu pakumvera coonadi kuti 6 mukakonde abale ndi cikondi cosanyenga, mukondane kweni kweni kucokera kumtima;

23 7 inu amene mudabadwanso, osati ndi mbeu yofeka, komatu yosaola, mwa mau a Mulungu amoyo ndi okhalitsa.

24 Popeza, 8 Anthu onse akunga udzu, Ndi ulemerero waowonse ngad duwa la udzu. Udzuwo ungotota, ndi duwa lace lingogwa;

25 9 Koma Mau a Mulungu akhala cikhalire. Ndipo 10 mau olalikidwa kwa Inu ndi jawo.

2

1 Momwemo pakutaya coipa conse, ndi cmyengo conse, ndi maonekedwe onyenga, ndi kadoka, ndi masiniiriro onse,

2 lirani monga makanda alero mkaka woyenera, wopanda cinyengo, kuti mukakule nao kufikira cipulumutso;

3 ngati mwalawa kuti Ambuye ali wokoma mtima;

4 amene pakudza kwa iye, mwala wamoyo, wokanidwatu ndi anthu, koma ndi Mulungu wosankhika, waulemu,

5 inunso ngati miyala yamoyo mumangidwa nyumba ya uzimu, kun mukhale ansembe oyera mtima, akupereka nsembe zauzimu, zolandiridwa ndi Mulungu mwa Yesu Kristu,

6 Cifukwa kwalembedwa m'lembo, Taona, ndiika m'Ziyoni mwala wotsiriza wa pangondya, wosankhika, wa mtengo wace; Ndipo wokhulupirira iye sadzanyazitsidwa.

7 Kwa inu tsono akukhulupira, ali wa mtengo wace; koma kwa iwo osakhulupira, Mwala umene omangawo anaukana, Womwewo unayesedwa mutu wa pangondya;

8 ndipo, Mwala wakukhumudwa nao, ndi thanthwe lopunthwitsa; kwa iwo akukhumudwa ndi mau, pokhala osamvera, kumenekonso adaikidwako.

9 Koma inu ndinu mbadwa yosankhika, ansembe acifumu, mtundu woyera mtima, anthu a mw ni wace, kotero kuti mukalakire zoposazo za iye amene anakuitanani muturuke mumdima, mulowe kuunika kwace kodabwitsa;

10 inu amene kale simunali anthu, koma tsopano muli anthu a Mulungu; amene kale simunalandira cifundo, koma tsopano mwalandira cifundo.

11 Okondedwa, ndikudandaulirani ngati alendo ndi ogonera mudzikanize zilakolako za thupi zimene zicita nkhondo pa moyo;

12 ndipo mayendedwe anu mwa amitundu akhale okoma, kuti, m'mene akamba za inu ngati ocita zoipa, akalemekeze Mulungu pakuona nchito zanu zabwino, m'tsiku la kuyang'anira.

13 Tadzigonjani kwa zoikika zonse za anthu, cifukwa ca Ambuye; ngakhale kwa mfumu, monga mutu wa onse;

14 kapena kwa akazembe, monga otumidwa ndi iye kukalanga ocira zoipa, koma kusimba ocita zabwino.

15 Pakuti cifuniro ca Mulungu citere, kuti ndi kucita zabwino mukatontholetse cipulukiro ca anthu opusa;

16 monga mfulu, koma osakhala nao ufulu monga cobisira coipa, koma ngati akapolo a Mulungu.

17 Citirani ulemu anthu onse. Kondani abale. Opani Mulungu, Citirani mfumu ulemu.

18 Anyamata inu, gonjerani ambuye anu ndi kuopa konse, osati abwino ndi aulere okha, komanso aukali.

19 Pakuti ici ndi cisomo ngati munthu, cifukwa ca cikumbu mtima pa Mulungu alola zacisoni, pakumva zowawa wosaziyenera.

20 Pakuti mbiri yokoma yanji, mukapirira pocimwa ndi kubwanyulidwapo? Komatu, ngati pocita zabwino, ndi kumvako zowawa mumapirira, kumeneko ndiko cisomo pa Mulungu.

21 Pakuti kudzacita ici mwaitanidwa; 1 pakutinso Kristu anamva zowawa m'malo mwanu, 2 nakusiyirani citsanzo kuti mnkalondole mapazi ace;

22 3 amene sanacita cimo, ndipo m'kamwa mwace sicinapezedwa cinyengo;

23 4 amene pocitidwa cipongwe sanabwezera cipongwe, pakumva zowawa, sanaopsa, koma 5 anapereka mlandu kwa iye woweruza kolungama;

24 6 amene anasenza macimo athu mwini yekha m'thupi mwace pamtanda, kuti ife, 7 titafa kumacimo, tikakhale ndi moyo kutsata cilungamo; 8 ameneyo mikwingwirima yace munaciritsidwa nayo.

25 Pakuti 9 munalikusocera ngati nkhosa; koma rsopano mwabwera kwa 10 Mbusa ndi Woyang'anira wa moyo wanu.

3

1 Momwemonso, akazi inu, mverani amuna anu ainu nokha; kuti, ngatinso ena samvera mau, akakodwe opanda mau mwa mayendedwe a akazi;

2 pakuona mayendedwe anu oyera ndi kuopa kwanu.

3 Amene kukometsera kwanu kusakhale kwa kunja, kuluka tsitsi ndi kubvala za golidi, kapena kubvala cobvala;

4 koma kukhale munthu wobisika wamtima, m'cobvala cosaola ca mzimu wofatsa ndi wacete, ndiwo wa mtengo wace wapatali pamaso pa Mulungu.

5 Pakuti koteronso kale akazi oyera mtima, akuyembekezera Mulungu, anadzikometsera okha, namvera amuna ao a iwo okha;

6 monga Sara anamvera Abrahamu, namucha iye mbuye; ameneyo mukhala ana ace ngati mucita bwino, osaopa coopsa ciri conse.

7 Momwemonso amuna inu, khalani nao monga mwa cidziwitso, ndi kucitira mkazi ulemu, monga cotengera cocepa mphamvu, monganso wolowa nyumba pamodzi wa cisomo ca moyo, kuti mapemphero anu angaletsedwe.

8 Cotsalira, khalani nonse a mdma umodzi, ocitirana cifundo, okondana ndi abale, acisoni, odzicepetsa:

9 osabwezera coipa ndi coipa, kapena cipongwe ndi cipongwe, koma penatu madalitso; pakuti kudzatsata ici mwaitanidwa, kuti mukalandire dalitso.

10 Pakuti, iye wofuna kukonda moyo, Ndi kuona masiku abwino, Aletse lilime lace lisanene coipa, Ndi milomo yace isalankhule cinyengo;

11 j Ndipo apatuke pacoipa, nacite cabwino; Afunefune mtendere ndi kuulondola.

12 Pakuti maso a Ambuye ali pa olungama, Ndi makutu ace akumva rembedzo lao; Koma nkhope ya Ambuye iri pa ocita zoipa,

13 Ndipo ndani iye amene adzakucitirani coipa, ngati mucita naco cangu cinthu cabwino?

14 Komatu ngatinso mukamva zowawa cifukwa ca cilungamo, odala inu; ndipo musaope pakuwaopa iwo, kapena musadere nkhawa;

15 koma mumpatulikitse Ambuye Kristu m'mitima yanu; okonzeka nthawi zonse kucita codzikanira pa yense wakukufunsani cifukwa ca ciyembekezo ciri mwa inu, komatu ndi cifatsondi mantha;

16 ndi kukhala naco cikumbu mtima cabwino, kuti umo akunenerani, iwo akunenera konama mayendedwe anu abwino m'Kristu akacitidwe manyazi.

17 Pakuti, kumva zowawa cifukwa ca kucita zabwino, ndi kumva zowawa cifukwa ca kucita zoipa, nkwabwino kumva zowawa cifukwa ca kucita zabwino, ngati citero cifuniro ca Mulungu,

18 Pakuti Kristunso adamva zowawa kamodzi, cifukwa ca macimo, wolungama m'malo mwa osalungama, kuti akatifikitse kwa Mulungu; wophedwatu m'thupi, koma woparsidwa moyo mumzimu;

19 m'menemonso anapita, nalalikira mizimu inali m'ndende,

20 imene inakhala yosamvera kale, pamene kuleza mtima kwa Mulungu kunalindira, m'masiku a Nowa, pokhala m'kukonzeka cingalawa, m'menemo owerengeka, ndiwo amoyo asanu ndi atatu, anapulumutsidwa mwa madzi;

21 cimenenso cifaniziro cace cikupulumutsani tsopano, ndico ubatizo, kosati kutaya kwa litsiro lace la thupi, komatu funso lace la cikumbu mtima cokoma kwa Mulungu, mwa kuuka kwa Yesu Kristu;

22 amene akhala pa dzanja lamanja la Mulungu, atalowa m'Mwamba; pali angelo, ndi maulamuliro, ndi zimphamvu, zomgonjera.

4

1 Popeza Kristu adamva zowawa m'thupi, mudzikonzere mtima womwewo; pakuti iye amene adamva zowawa m'thupi walekana nalo cimo;

2 kuti nthawi yotsalira simukakhalenso ndi moyo m'thupi kutsata zilakolako za anthu, koma cifuniro ca Mulungu.

3 Pakuti nthawi yapitayi idatifikira kucita cifuno ca amitundu, poyendayenda ife m'kukhumba zonyansa, zilakolako, maledzero, madyerero, mamwaimwa, ndi kupembedza mafano kosaloleka;

4 m'menemo ayesa ncacilendo kuti simuthamanga nao kufikira kusefukira komwe kwa citayiko, nakucitirani mwano;

5 amenewo adzamwerengera iye wokhala wokonzeka kuweruza amoyo ndi akufa.

6 Pakuti cifukwa ca ici walalikidwa Uthenga Wabwino kwa iwonso adafawo, kuti akaweruzidwe monga mwa anthu m'thupi, koma akakhale ndi moyo monga mwa Mulungu mumzimu.

7 Koma citsiriziro ca zinthu zonse ciri pafupi; cifukwa cace khalani anzeru, ndipo dikirani m'mapemphero;

8 koposa zonse mukhale naco cikondano ceni ceni mwa inu nokha; pakuti cikondano cikwiriritsa unyinji wa macimo;

9 mucerezane wina ndi mnzace, osadandaula:

10 monga yense walandira mphatso, mutumikirane nayo, ngati adindo okoma a cisomo ca mitundu mitundu ca Mulungu;

11 akalankhula wina, alankhule ngati manenedwe a Mulungu; wina akatumikira, acite ngati mu mphamvu imene Mulungu ampatsa, kuti m'zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Kristu, amene ali nao ulemerero ndi mphamvu ku nthawi za nthawi. Amen.

12 Okondedwa, musazizwe ndi mayesedwe amoto adakugwerani inu akhale cakukuyesani, ngati cinthu cacilendo cacitika nanu:

13 koma popeza mulawana ndi Kristu zowawa zace, kondwerani; kutinso pa bvumbulutso la ulemerero wace mukakondwere kwakukurukuru.

14 Mukatonzedwa pa dzina la Kristu, odala inu; pakuti Mzimu wa ulemerero, ndi Mzimu wa Mulungu apuma pa inu.

15 Pakuti asamve zowawa wina wa inu ngati wambanda, kapena mbala, kapena wocita zoipa, kapena ngati wodudukira;

16 koma akamva zowawa ngati Mkristu asacite manyazi; koma alemekeze Mulungu m'dzina ili.

17 Cifukwa yafika nthawi kuti ciweruziro ciyambe pa nyumba ya Mulungu; komangati ciyamba ndi ife, citsiriziro ca iwo osamvera Uthenga Wabwino wa Mulungu cidzakhala ciani?

18 Ndipo ngati munthu wolungama apulumuka ndi kuyesetsa kokha kokha, munthu wosapembedza ndi wocimwa adzaoneka kuti?

19 Koteronso iwo akumva zowawa monga mwa cifuniro ca Mulungu aike moyo wao ndi kucita zokoma m'manja a Wolenga wokhulupirika.

5

1 Akulu tsono mwa inu ndiwadandaulira, ine mkulu mnzanu ndi mboni ya zowawa za Kristu, ndinenso wolawana nao ulemerero udzabvumbulutsikawo:

2 Wetani gulu la Mulungu liri mwa inu, ndi kuliyang'anira, osati mokangamiza, koma mwaufulu, kwa Mulungu; osatsata phindu lonyansa, koma mwacangu;

3 osati monga ocita ufumu pa iwo a udindo wanu, koma okhala zitsanzo za gululo.

4 Ndipo pakuonekera Mbusa wamkulu, mudzalandira korona wa ulemerero, wosafota. Momwemonso, anyamata inu, mverani akulu.

5 Koma nonsenu mubvale kudzicepetsa kuti mutumikirane; pakuti Mulungu akaniza odzikuza, koma apatsa cisomo kwa odzicepetsa.

6 Potero dzicepetseni pansi pa dzanja la mphamvu lao Mulungu, kuti panthawi yace akakukwezeni;

7 ndi kutaya pa iye nkhawa yanu yonse, pakuti iye asamalira inu.

8 Khalani odzisungira, dikirani; mdani wanu mdierekezi, monga mkango wobuma, ayendayenda ndi kufunafuna wina akamlikwire:

9 ameneyo mumkanize okhazikika m'cikhulupiriro, podziwa kuti zowawa zomwezo zirimkukwaniridwa pa abale anu ali m'dziko.

10 Ndipo Mulungu wa cisomo conse, amene adakuitanani kulowa ulemerero wace wosatha mwa Kristu, mutamva zowawa kanthawi, adzafikitsa inu opanda cirema mwini wace, adzakhazikitsa, adzalimbikitsa inu.

11 Kwa iye kukhale mphamvu ku nthawi za nthawi. Amen.

12 Mwa Silvano, mbale wathu wokhulupirika monga ndimayesa, ndalembera kwa inu mwacidule, ndi kudandaulira, ndi kucita umboni, kuti cisomo coona ca Mulungu ndi ici; m'cimeneci muimemo.

13 Iye wa ku Babulo wosankhidwa pamodzi nanu akulankhulani; ateronso Marko mwana wanga.

14 Lankhulanani ndi cipsompsono ca cikondi. Mtendere ukhale ndi inu nonse muli mwa Kristu.