1

1 MAU a Nehemiya mwana wa Hakaliya. Kunali tsono mwezi wa Kisilevi, caka ca makumi awiri, pokhala ine ku Susani ku nyumba ya mfumu,

2 anafika Hanani, mmodzi wa abale anga, iye ndi amuna ena a ku Yuda; ndipo ndinawafunsa za Ayuda adapulumukawo otsala andende, ndi za Yerusalemu.

3 Nanena nane iwo, Otsalawo otsala andende uko ku dzikoko akulukutika kwakukuru, nanyozedwa; ndi linga la Yerusalemu lapasuka, ndi zipata zace zatenthedwa ndi moto.

4 Ndipo kunali, pakumva'mau awa, ndinakhala pansi ndi kulira misozi, ndi kucita maliro masiku ena, ndinasalanso, ndi kupemphera pamaso pa Mulungu wa Kumwamba,

5 ndi kuti, Ndikupembedzani Yehova, Mulungu wa Kumwamba, Mulungu wamkuru ndi woopsa, wakusunga pangano ndi cifundo ndi iwo akumkonda ndi kusunga malamulo ace;

6 muchere khutu, ndi maso anu atseguke kumvera pemphero la kapolo wanu, ndilipempha pamaso panu tsopano apa msana ndi usiku, kupempherera ana a Israyeli akapolo anu, ndi kuulula zoipa za ana a Israyeli zimene tacimwira nazo Inu; inde tacimwa, ine ndi nyumba ya atate wanga.

7 Tacita mwamphulupulu pa Inu, osasunga malamulo, kapena malemba, kapena maweruzo, amene mudalamulita mtumiki wanu Mose.

8 Mukumbukile mau mudalamulira mtumiki wanu Mose, ndi kuti, Mukalakwa, ndidzakubalalitsani mwa mitundu ya anthu;

9 koma mukabwerera kudza kwa Ine, ndi kusunga malamulo anga, ndi kuwacita, angakhale otayika anu anali ku malekezero a thambo, ndidzawasonkhanitsa kucokera komweko, ndi kubwera nao ku malo ndinawasankha kukhalitsako dzina langa.

10 Ndipo awa ndi akapolo anu ndi anthu anu, amene munawaombola ndi mphamvu yanu yaikuru, ndi dzanja lanu lolimba.

11 Yehova, mucherere khutu pemphero la kapolo wanu, ndi pemphero la akapolo anu okondwera nako kuopa dzina lanu; ndipo mulemereze kapolo wanu lero lino, ndi kumuonetsera cifundo pamaso pa munthu uyu. Koma ndinali ine wothirira mfumu cakumwa cace.

2

1 Koma kunacitika mwezi wa Nisana, caka ca makumi awiri ca Aritasasta mfumu pokhala vinyo pamaso pace, ndinatenga vinyoyo ndi kuipatsa mfumu. Koma sindidakhala wacisoni pamaso pace ndi kale lonse.

2 Ninena nane mfumu, Nkhope yako nja cisoni cifukwa ninji popeza sudwala? ici si cinthu cina koma cisoni ca mtima. Pamenepo ndinacita mantha akuru.

3 Ndipo ndinati kwa mfumu, Mfumu ikhale ndi moyo kosatha; ilekerenji nkhope yanga kucita cisoni, popeza pali bwinja kumudzi kuli manda a makolo anga, ndi zipata zace zopsereza ndi moto.

4 Ndipo mfumu inati kwa ine, Ufunanji iwe? Pamenepo ndinapemphera Mulungu wa Kumwamba.

5 Ndipo ndinati kwa mfumu, Cikakomera mfumu, ndi mtima wanu ukakomera kapolo wanu, munditumize ku Yuda ku mudzi wa manda a makolo anga, kuti ndiumange.

6 Ninena nane mfumu, irikukhala pansi pamodzi ndi mkazi wace wamkuru, Ulendo wako ngwa nthawi yanji, udzabweranso liti? Ndipo kudakonda mfumu kunditumiza nditaichula nthawi.

7 Ndinanenanso kwa mfumu, Cikakomera mfumu, indipatse akalata kwa ziwanga za tsidya lija la mtsinje, andilole ndipitirire mpaka ndifikira ku Yuda;

8 ndi kalata kwa Asafu wosunga misitu ya mfumu, kuti andipatse mitengo ya mitanda ya ku zipata, za linga liri kukacisi, ndi ya linga la mudzi, ndi ya nyumba imene ndidzalowamo ine. Ndipo mfumu inandipatsa monga mwa dzanja lokoma la Mulungu londikhalira.

9 Ndinafika tsono kwa ziwanga za tsidya lino la mtsinje, ndipo ndinawapatsa akalata a mfumu. Koma mfumu idatumiza apite nane akazembe a nkhondo, ndi apakavalo.

10 Atamva Sanibalati Mhoroni, ndi Tobiya kapoloyo M-amoni, cidawaipira kwakukuru, kuti wadza munthu kuwafunica ana a Israyeli cokoma.

11 Motero ndinafika ku Yerusalemu, ndi kukhalako masiku atatu.

12 Ndipo ndinauka usiku, ine ndi amuna owerengeka nane, osauza munthu yense ine coika Mulungu wanga m'mtima mwanga ndicitire Yerusalemu; panalibenso nyama yina nane, koma nyama imene ndinakhalapo.

13 Ndipo ndinaturuka usiku pa cipata ca kucigwa, kumka ku citsime ca cinjoka, ndi ku cipata ca kudzala, ndi kuyang'ana malinga a Yerusalemu adapasukawo, ndi zipata zace zothedwa ndi moto.

14 Ndipo ndinapitima kumka ku cipata cacitsime, ndi ku dziwe la mfumu; koma popita nyama iri pansi panga panaicepera.

15 Ndipo ndinakwera usiku kumtsinje, ndi kuyang'ana lingali; ndinabwerera tsono ndi kulowa pa cipata ca kucigwa, momwemo ndinabwereranso.

16 Koma olamulira sanadziwa uko ndinamuka, kapena cocita ine; sindidauzenso kufikira pamenepo Ayuda, kapena ansembe, kapena aufuru, kapena olamulira, kapena otsala akucita nchitoyi.

17 Pamenepo ndinanena nao, Muona coipa m'mene tirimo, kuti Yerusalemu ali bwinja, ndi zipata zace zotentha ndi moto; tiyeni, timange linga la Yerusalemu, tisakhalenso cotonzedwa.

18 Ndinawauzanso za dzanja la Mulungu wanga londikhalira mokoma, ndiponso za mau anandiuza mfumu. Nati iwo, Tinyamuke, timange. Cotero anandilimbitsira manja mokoma.

19 Koma Sanibalati Mhoroni, ndi Tobiya kapolo M-amoniyo, ndi Gesemu M-arabu, anamva natiseka pwepwete, natipeputsa, nati, Ciani ici mucicita? Mulikupandukira mfumu kodi?

20 Koma ndinawabwezera mau, ndi kunena nao, Mulungu Wam'mwamba, Iye ndiye adzatilemeza; cifukwa cace ife akapolo ace tidzanyamuka ndi kumanga; koma inu mulibe gawo, kapena ulamuliro, kapena cikumbukilo, m'Yerusalemu.

3

1 Pamenepo Eliasibu mkuru wa ansembe ananyamuka pamodzi ndi abale ace ansembe, namanga cipata cankhosa; anacipatula, naika zitseko zace, inde anacipatula mpaka nsanja ya Mea, mpaka nsanja ya Hananeeli.

2 Ndi pambali pace anamanga amuna a ku Yeriko. Ndi pambali pao anamanga Zakuri mwana wa Imri.

3 Ndi cipata cansomba anacimanga ana a Hasenaa; anamanga mitanda yace, ndi kuika zitseko zace, zokowera zace, ndi mipingiridzo yace.

4 Ndi pambali pao anakonza Meremoti mwana wa Uliya, mwana wa Kozi. Ndi pambali pao anakonza Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabele. Ndi pambali pao anakonza Zadoki mwana wa Baana.

5 Ndi pambali pao anakonza Atekoa; koma omveka ao sanapereka makosi ao ku nchito ya Mbuye wao.

6 Ndi cipata cakale anacikonza Yoyada mwana wa Paseya; ndi Mesulamu mwana wa Besodeya anamanga mitanda yace, ndi kuika zitseko zace, ndi zokowera zace, ndi mipingiridzo yace.

7 Ndi pambali pao anakonza Melatiya Mgibeoni, ndi Yadoni Mheronoti, ndi amuna a ku Gibeoni, ndi a ku Mizipa, wa ulamuliro wa ciwanga tsidya lino la mtsinje.

8 Pambali pace anakonza Uziyeli mwana wa Haraya, wa iwo osula golidi. Ndi padzanja pace anakonza Hananiya, wa iwo osanganiza zonunkhira; nalimbikitsa Yerusalemu mpaka linga lacitando.

9 Ndi pambali pao anakonza Refaya mwana wa Huri, ndiye mkuru wa dera lina la dziko la Yerusalemu.

10 Ndi pambali pao anakonza Yedaya mwana wa Harumafi, pandunji pa nyumba yace. Ndi pambali pace anakonza Hatusi mwana wa Hasabineya.

11 Malikiya mwana wa Harimu, ndi Hasubi mwana wa Pahati-Moabu, anakonzal gawo lina, ndi nsanja ya ng'anjo.

12 Ndi pambali pace anakonza Salumu mwana wa Halohesi, mkuru wa dera lina la dziko la Yerusalemu, iye ndi ana ace akazi.

13 Cipata ca kucigwa anacikonza Hanini; ndi okhala m'Zanowa anacimanga, naika zitseko zace, zokowera zace, ndi mipiringidzo yace; ndiponso mikono cikwi cimodzi ca lingalo mpaka ku cipata ca kudzala.

14 Ndi cipata ca kudzala anacikonza Malikiya mwana wa Rekabu, mkuru wa dziko la Bete Hakeremu; anacimanga, naika zitseko zace, zokowera zace, ndi mipiringidzo yace.

15 Ndi cipata ca kukasupe anacikonza Saluni mwana wa Koli, Hoze mkuru wa dziko la Mizipa anacimanga, nacikomaniza pamwamba pace, naika zitseko zace, zokowera zace, ndi mipiringidzo yace; ndiponso linga la dziwe la Sela pa munda wa mfumu, ndi kufikira ku makwerero otsikira ku mudzi wa Davide.

16 Potsatizana naye anakonza Nehemiya mwana wa Azibuki, mkuru wa dera lace lina la dziko la Bete Zuri, mpaka malo a pandunji pa manda a Davide, ndi ku dziwe adalikumba, ndi ku nyumba ya amphamvu aja.

17 Potsatizana naye anakonza Alevi, Rehumu mwana wa Bani. Pambali pace anakonza Hasabiya mkuru wa dera lina la dziko la Keila, kukonzera dziko lace.

18 Potsatizana naye anakonza abale ao, Bavai mwana wa Henadadi, mkuru wa dera lina la dziko la Keila.

19 Ndi pa mbali pace Ezeri mwana wa Yesuwa, mkuru wa Mizipa, anakonza gawo lina, pandunji pokwerera ku nyumba yosungamo zida za nkhondo, popindirira linga.

20 Potsatizana naye Baruki mwana wa Zabai anafulumira kukonza gawo lina kuyambira popindirira mpaka ku khomo la nyumba ya Eliasibu mkuru wa ansembe.

21 Potsatizana naye Meremoti mwana wa Uliya mwana wa Hakozi anakonza gawo lina, kuyambira ku khomo la nyumba ya Eliasibu kufikira malekezero ace a nyumba ya Eliasibu.

22 Ndi potsatizana naye anakonza ansembe okhala kucidikha.

23 Potsatizana nao anakonza Benjamini ndi Hasubi pandunji pa nyumba pao, Potsatizana nao anakonza Azariya mwana wa Maseya mwana wa Ananiya pafupi pa nyumba yace.

24 Potsatizana naye Binui mwana wa Henadadi anakonza gawo lina, kuyambira ku nyumba ya Azariya kufikira popindirira kufikira kungondya.

25 Palali mwana wa Uzai anakonza pandunji popindirira, ndi nsanja yosomphoka pa nyumba ya mfumu ya kumtunda, imene iri ku bwalo la kaidi. Potsatizana naye anakonza Pedaya mwana wa Parosi.

26 Koma Anetini okhala m'Ofeli anakonza kufikira ku malo a pandunji pa cipata ca kumadzi kum'mawa, ndi nsanja yosomphokayo,

27 Potsatizana nao Atekoa anakonza gawo lina, pandunji pa nsanja yaikuru yosomphoka ndi ku linga la Ofeli.

28 Kumtunda kwa cipata ca akavalo anakonza ansembe, yense pandunji pa nyumba yace.

29 Potsatizana nao anakonza Zadoki mwana wa Imeri pandunji pa nyumba yace. Ndi potsatizana naye anakonza Semaya mwana wa Sekaniya, wosunga cipata ca kum'mawa.

30 Potsatizana naye Hananiya mwana wa Selemiya, ndi Hanuni mwana wacisanu ndi cimodzi wa Salafi, anakonza gawo lina. Potsatizana naye anakonza Mesulamu mwana wa Berekiya pandunji pa cipinda cace.

31 Potsatizana naye anakonza Malikiya wina wa osula golidi kufikira ku nyumba ya Anetini, ndi ya ocita malonda, pandunji pa cipata ca Hamifikadi, ndi ku cipinda cosanja ca kungondya.

32 Ndi pakati pa cipinda cosanja ca kungondya ndi cipata cankhosa anakonza osula golidi ndi ocita malonda.

4

1 Ndipo kunali, atamva Sanibalati kuti tinalikumanga lingali, kudamuipira, nakwiya kwakukuru, naseka Ayuda pwepwete.

2 Nanena iye pamaso pa abale ace ndi ankhondo a ku Samariya, nati, Alikucitanji Ayuda ofokawa? adzimangire linga kodi? adzapereka nsembe kodi? adzatsiriza tsiku limodzi kodi? adzakometsanso miyala ya ku miunda yotenthedwa?

3 Ndipo Tobiya M-amoni anali naye, nati, Cinkana ici acimanga, ikakwerako nkhandwe, idzagamula linga lao lamiyala.

4 Imvani, Mulungu wathu, popeza tanyozeka ife; muwabwezere citonzo cao pamtu pao, ndi kuwapereka akhale cofunkhidwa m'dziko la ndende;

5 ndipo musakwirira mphulupulu yao, ndi kulakwa kwao kusafafanizike pamaso panu; pakuti anautsa mkwiyo wanu pamaso pa omanga linga.

6 Koma tinamanga lingali, ndi linga lonse linalumikizana kufikira pakati mpakati; popeza mitima ya anthu inalunjika kunchito.

7 Koma kunali, atamva Sanibalati, ndi Tobiya, ndi Aarabu, ndi Aamoni, ndi Aasidodi, kuti makonzedwe a malinga a Yerusalemu anakula, ndi kuti mopasuka mwace munayamba kutsekeka, cidawaipira kwambiri;

8 napangana ciwembu iwo onse pamodzi, kudzathira nkhondo ku Yerusalemu, ndi kucita cisokonezo m'menemo.

9 Koma tinapemphera kwa Mulungu wathu, ndi kuwaikira olindirira usana ndi usiku, cifukwa ca iwowa.

10 Ndipo Ayuda anati, Mphamvu ya osenza akatundu yatha, ndi dothi licuruka, motero sitidzakhoza kumanga lingali.

11 Nati adani athu, Sadzadziwa kapena kuona mpaka talowa pakati pao, ndi kuwapha, ndi kuleketsa nchitoyi.

12 Ndipo kunali, atafika Ayuda okhala pafupi pao ocokera pamalo ponse, anatiuza ife kakhumi, Bwererani kwa ife.

13 Cifukwa cace ndinawaika potera m'kati mwa linga, popenyeka; inde ndinaika anthu monga mwa mabanja ao, akhale nao malupanga ao, nthungo zao, ndi mauta ao.

14 Ndipo ndinapenya, ndinanyamuka, ndinanena kwa aufulu, ndi olamulira, ndi anthu otsala, Musamawaopa iwo; kumbukilani Yehova wamkuru ndi woopsa, ndi kuponyera nkhondo abale anu, ana anu amuna ndi akazi, akazi anu, ndi nyumba zanu.

15 Ndipo kunali, pakumva adani athu kuti cinadziwika nafe, ndi kuti Mulungu adapititsa pacabe uphungu wao, tinabwera tonse kumka kulinga, yense ku nchito yace.

16 Ndipo kuyambira pamenepo gawo lina la anyamata anga anagwira nchito, ndi gawo ina linagwira nthungo, zikopa, ndi mauta, ndi maraya acitsulo; ndi akuru anali m'mbuyo mwa nyumba yonse ya Yuda.

17 Iwo omanga linga, ndi iwo osenza katundu, posenza, anacita ali yense ndi dzanja lace lina logwira nchito, ndi lina logwira cida;

18 ndi omanga linga ali yense anamangirira lupanga lace m'cuuno mwace, nagwira nchito motero. Ndipo woomba lipenga anali ndi ine.

19 Ndipo ndinati kwa aufulu, ndi olamulira, ndi anthu otsala, Nchito ndiyo yocuruka ndi yacitando, ndi ife tiri palace palace palingapo, yense azana ndi mnzace;

20 pali ponse mukumva mau a lipenga, musonkhanire komweko kwa ife; Mulungu wathu adzatigwirira nkhondo.

21 Momwemo tinalikugwira nchito; gawo lina la iwo linagwira nthungo kuyambira mbanda kuca mpaka zaturuka nyenyezi.

22 Ndinanenanso kwa anthu nthawi yomweyi, Ali yense agone m'Yerusalemu pamodzi ndi mnyamata wace, kuti atilindirire usiku, ndi kugwira nchito usana.

23 Ndipo ine, ndi abale anga, ndi anyamata anga, angakhale amuna olindirira onditsata ine, nnena mmodzi yense wa ife anabvula zobvala zace, yense anapita ndi cida cace kumadzi.

5

1 Pamenepo panamveka kulira kwakukuru kwa anthu ndi akazi ao kudandaula pa abale ao Ayuda.

2 Popeza panali ena akuti, Ife, ana athu amuna ndi akazi, ndife ambiri; talandira tirigu, kuti tidye tikhale ndi moyo.

3 Panali enanso akuti, Tirikupereka cikole minda yathu, ndi minda yathu yampesa ndi nyumba zathu; kuti tilandire tirigu cifukwa ca njalayi.

4 Panali enanso akuti, Takongola ndarama za msonkho wa mfumu; taperekapo cikole minda yathu, ndi minda yathu yampesa.

5 Koma tsopano thupi lathu likunga thupi la abale athu, ana athu akunga ana ao; ndipo taonani, titengetsa ana athu amuna ndi akazi akhale akapolo, ndi ana athu akazi ena tawatengetsa kale; ndipo tiribe ife mphamvu ya kucitapo kanthu; ndi minda yathu, ndi minda yathu yampesa, nja ena.

6 Ndipo pakumva kulira kwao, ndi mau ao, kunandiipira kwambiri.

7 Pamenepo mtima wanga unandipangira; ndipo ndinatsutsana nao aufuru ndi olamulira, ndi kunena nao, Mukongoletsa mwa phindu yense kwa mbale wace. Ndipo ndinasonkhanitsa msonkhano waukuru wakuwatsutsa.

8 Ndipo ndinanena, nao, Ife monga umo tinakhoza, tinaombola abale athu Ayuda ogulitsidwa kwa amitundu; ndipo kodi inu mukuti mugulitse abale anu, kapena tiwagule ndi ife? Pamenepo anakhala du, nasowa ponena.

9 Ndinatinso, Cinthu mucitaci si cokoma ai; simuyenera kodi kuyenda m'kuopa Mulungu wathu, cifukwa ca mnyozo wa amitundu, ndiwo adani athu?

10 Kodi ine, ndi abale anga, ndi anyamata anga, tiwakongoletsa ndarama ndi tirigu mwa phindu? Ndikupemphani, tileke phindu ili.

11 Abwezereni lero lomwe minda yao, minda yao yampesa, minda yao yaazitona, ndi nyumba zao, ndi limodzi la magawo zana limodzi la ndarama, ndi tirigu, vinyo, ndi mafuta, limene muwalipitsa.

12 Pamenepo anati, Tidzawabwezera osawalipitsa kanthu, tidzacita monga momwe mwanena. Pamenepo ndinaitana ansembe, ndi kuwalumbiritsa, kuti adzacita monga mwa mau awa.

13 Ndinakutumulanso maraya anga, ndi kuti, Mulungu akutumule momwemo munthu yense wosasunga mau awa, ku nyumba yace, ndi ku nchito yace; inde amkutumule momwemo, namtayire zace zonse. Ndi msonkhano wonse unati, Amen, nalemekeza Yehova. Ndipo anthu anacita monga mwa mau awa.

14 Ndipo ciyambire tsiku lija anandiika ndikhale kazembe wao m'dziko la Yuda; kuyambira caka ca makumi awiri kufikira caka ca makumi atatu mphambu ziwiri ca Aritasasta mfumu, ndizo zaka khumi ndi ziwiri, ine ndi abale anga sitinadya cakudya ca kazembe.

15 Koma akazembe akale ndisanakhale ine, analemetsa anthu, nadzitengera kwa iwo mkate, ndi vinyo, pamodzi ndi siliva masekeli makumi anai; angakale anyamata ao anacita ufumu pa anthu; koma sindinatero ine, cifukwa ca kuopa Mulungu.

16 Ndiponso ndinalimbikira nchito ya linga ili, ngakhale dziko sitinaligula, ndi anyamata anga onse anasonkhanira nchito komweko.

17 Panalinso podyera ine Ayuda ndi olamulira amuna zana limodzi; mphambu makumi asanu, pamodzi ndi iwo akutidzera kucokera kwa amitundu otizinga.

18 Zokonzekeratu tsiku limodzi tsono ndizo ng'ombe imodzi, ndi nkhosa zonenepa zisanu ndi imodzi, anandikonzeratunso nkhuku, ndi kamodzi atapita masiku khumi vinyo wambiri wa mitundu mitundu; cinkana conseci sindinafunsira cakudya ca kazembe, popeza ukapolo unalemerera anthuwo.

19 Mundikumbukire Mulungu, zindikomere zonse ndinacitira anthu awa.

6

1 Kunali tsono, atamva Sanibalati, ndi Tobiya, ndi Gesemu M-arabu, ndi adani athu otsala, kuti ndidatha kumanga lingali, posatsalaponso popasuka; (ngakhale pajapo sindinaika zitseko pazipata);

2 anatumiza mau kwa ine Sanibalati ndi Gesemu, kuti, Tiyeni tikomane ku midzi ya ku cigwa ca Ono; koma analingirira za kundicitira coipa.

3 Ndipo ndinawatumizira mithenga, ndi kuti, Ndirikucita nchito yaikuru, sindikhoza kutsika; ndiidulirenji padera nchito poileka ine, ndi kukutsikirani?

4 Nanditumizira ine mau otere kanai; ndinawabwezeranso mau momwemo.

5 Pamenepo Sanibalati anatuma mnyamata wace kwa ine kacisanu, ndi kalata wosatseka m'dzanja mwace;

6 m'menemo mudalembedwa, Kwamveka mwa amitundu, ndi Gasimu acinena, kuti iwe ndi Ayuda mulikulingirira za kupanduka; cifukwa cace mulikumanga lingali; ndipo iwe udzakhala mfumu yao monga mwa mau awa.

7 Ndiponso waika aneneri akubukitsa za iwe ku Yerusalemu, ndi kuti, Ku Yuda kuli mfumu, ndipo zidzamveka kwa mfumu, kuti kuli zotere. Tiyeni tsono tipangane pamodzi.

8 Koma ndinamtumizira mau, akuti, Palibe zinthu zotere zonga unenazi, koma uzilingirira mumtima mwako.

9 Pakuti anafuna onse kutiopsa, ndi kuti, Manja ao adzaleka nchito, ndipo siidzacitika. Koma Inu, Mulungu, mulimbitse manja anga tsopano.

10 Pamenepo ndinalowa m'nyumba ya Semaya mwana wa Delaya, mwana wa Mehetabele, wobindikizidwayo, ndipo anati, Tikomane ku nyumba ya Mulungu m'kati mwa Kacisi, titsekenso pa makomo a Kacisi; pakuti akudza kudzapha iwe, inde akudza usiku kudzapha iwe.

11 Koma ndinati, Munthu ngati ine nkuthawa kodi? ndani wonga ine adzalowa m'Kacisi kupulumutsa moyo wace? sindidzalowamo.

12 Ndipo ndinazindikira kuti sanamtuma Mulungu; koma ananena coneneraco pa ine, popeza Tobiya ndi Sanibalati adamlembera.

13 Anamlembera cifukwa ca ici, kuti ine ndicite mantha, ndi kucita cotero, ndi kucimwa; ndi kuti anditolerepo mbiri yoipa ndi kundinyoza.

14 Mukumbukile, Mulungu wanga, Tobiya ndi Sanibalati monga mwa nchito zao izi, ndi Nowadiya mneneri wamkazi yemwe, ndi aneneri otsala, amene anafuna kundiopsa.

15 Ndipo linga linatsirizika pa tsiku la makumi awiri ndi lacisanu la mwezi wa Eluli, titalimanga masiku makumi asanu mphambu awiri.

16 Ndipo kunali atacimva adani athu onse, amitundu onse akutizinga anaopa, nagwadi nkhope; popeza anazindikira kuti nchitoyi inacitika ndi Mulungu wathu.

17 Masikuwo aufulu a Yuda analemberanso akalata ambiri kwa Tobiya; ndipo anawafikanso akalata ace a Tobiya.

18 Pakuti ambiri m'Yuda analumbirirana naye cibwenzi; popeza ndiye mkamwini wace wa Sekaniya mwana wa Ara; ndi mwana wace Yehohanana adadzitengera mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya.

19 Anachulanso nchito zace zokoma pamaso panga namfotokozera iye mau anga. Ndipo Tobiya anatumiza akalata kuti andiopse ine.

7

1 Ndipo atatha kumanga linga, ndinaika zitseko, nakhazika odikira, ndi oyimbira, ndi Alevi;

2 ndipo ndinawapatsa mbale wanga Hanani, ndi Hananiya kazembe wa kuboma, ulamuliro wa pa Yerusalemu; popeza ndiye munthu wokhulupirika, naposa ambiri pakuopa Mulungu.

3 Ndinanenanso nao, Asatsegule pa zipata za Yerusalemu lisanafunde dzuwa; ndi poimirira odikira atseke pazipata, nimuzipiringidze, nimuike alonda mwa iwo okhala m'Yerusalemu, yense polindirira pace, yense pandunji pa nyumba yace.

4 Mudziwo tsono ndi wacitando, ndi waukuru; koma anthu anali m'mwemo ngowerengeka, nyumba zomwe sizinamangike.

5 Ndipo Mulungu wanga anaika m'mtima mwanga kuti ndiwasonkhanitse aufuru, ndi olamulira, ndi anthu, kuti awerengedwe mwa cibadwidwe cao. Ndipo ndinapeza buku la cibadwidwe la iwo adakwerako poyamba paja; ndinapeza mudalembedwa m'mwemo.

6 Ana a dziko amene anakwera kucokera kundende a iwo adatengedwa ndende, amene Nebukadinezara mfumu ya Babulo adawatenga, anabwera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, yense ku mudzi wace, ndi awa:

7 ndiwo amene anadza ndi Zerubabele: Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Moredekai, Bilisani, Misiperete, Bigivai, Nehumu, Baana. Mawerengedwe a amuna a anthu Aisrayeli ndiwo:

8 ana a Parosi zikwi ziwiri mphambu zana limodzi kudza makumi asanu ndi awiri.

9 Ana a Sefatiya, mazana atatu mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.

10 Ana a Ara, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.

11 Ana a Pakati Moabu, a ana a Yesuwa ndi Yoabu, zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi atatu kudza khumi limodzi ndi asanu ndi atatu.

12 Ana a Elamu, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri ndi makumi asanu kudza anai.

13 Ana a Zatu, mazana asanu ndi atatu mphambu makumi anai kudza asanu.

14 Ana a Zakai, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi asanu ndi limodzi.

15 Ana a Binui, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi anai kudza asanu ndi atatu.

16 Ana a Betai, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.

17 Ana a Azigadi, zikwi ziwiri mphambu mazana atatu kudza makumi awiri ndi awiri.

18 Ana a Adonikamu, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi limodzi, kudza asanu ndi awiri.

19 Ana a Bigivai, zikwi ziwiri mphambu makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi awiri.

20 Ana a Adini, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu kudza asanu.

21 Ana a Aberi, a Hezekiya, makumi asanu ndi anai kudza asanu ndi atatu.

22 Ana a Hasumu, mazana atatu mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.

23 Ana a Bezai, mazana atatu mphambu makumi awiri kudza anai.

24 Ana a Harifi, zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.

25 Ana a Gibeoni, makumi asanu ndi anai kudza asanu.

26 Amuna a ku Betelehemu ndi ku Netofa, zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu kudza asanu ndi atatu.

27 Amuna a ku Anatoti, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.

28 Amuna a ku Bete-Azimaveti, makumi anai kudza awiri.

29 Amuna a ku Kiriyati Yearimu, Kefiira, ndi Beeroti, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi anai kudza atatu.

30 Amuna a ku Rama ndi Geba, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza mmodzi.

31 Amuna a ku Mikimasi, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza awiri.

32 Amuna a ku Betele ndi Ai, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza atatu.

33 Amuna a ku Nebo winayo, makumi asanu kudza awiri.

34 Ana a Elamu winayo, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri ndi makumi asanu kudza anai.

35 Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.

36 Ana a Yeriko, mazana atatu mphambu makumi anai kudza asanu.

37 Ana a Lodi, Hadidi, ndi Ono, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi awiri kudza mmodzi.

38 Ana a Senaa, zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi anai kudza makumi atatu.

39 Ansembe: ana a Yedaya, a nyumba ya Yesuwa, mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu ndi awiri kudza atatu.

40 Ana a Imeri, cikwi cimodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.

41 Ana a Pasuru, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri kudza makumi anai ndi asanu ndi awiri.

42 Ana a Harimu, cikwi cimodzi mphambu khumi limodzi kudza asanu ndi awiri.

43 A Levi: ana a Yesuwa, a Kadimiyeli, a ana a Hodeva, makumi asanu ndi awiri kudza anai.

44 Oyimbira: ana a Asafu, zana limodzi mphambu makumi anai kudza asanu ndi atatu.

45 Odikira: ana a Salumu, ana a Ateri, ana a Talimoni, ana a Akubu, ana a Hatita, ana a Sobai, zana limodzi mphambu makumi atatu kudza asanu ndi atatu.

46 Anetini: ana a Ziha, ana a Hasufa, ana a Tabaoti,

47 ana a Kerosi, ana a Siya, ana a Padoni,

48 ana a Lebana, ana a Hagaba, ana a Salimai,

49 ana a Hanani, ana a Gideri, ana a Gahara,

50 ana a Reaya, ana a Rezini, ana a Nekoda,

51 ana a Gazamu, ana a Uza, ana a Paseya,

52 ana a Besai, ana a Meunimu, ana a Nefusesimu,

53 ana a Bakibuki, ana a Hakufa, ana a Harihuri,

54 ana a Baziliti, ana a Mehida, ana a Harisa,

55 ana a Barikosi, ana a Sisera, ana a Tema,

56 ana a Neziya, ana a Hatifa.

57 Ana a akapolo a Solomo: ana a Sotai, ana a Sofereti, ana a Perida,

58 ana a Yaala, ana a Darikoni, ana a Gideli,

59 ana a Sefatiya, ana a Hatili, ana a Pokereti Hazebaimu, ana a Amoni.

60 Anetini onse, ndi ana a akapolo a Solomo, ndiwo mazana atatu mphambu makumi asanu ndi anai kudza awiri.

61 Ndipo okwera kucokera ku Telemela, Teleharisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, ndi awa; koma sanakhoza kuchula nyumba za makolo ao, kapena mbumba zao, ngati ali a Israyeli;

62 ana a Delaya, ana a Tobiya, ana a Nekoda, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi anai kudza awiri.

63 Ndi a ansembe: ana a Hobaya, ana a Hokozi, ana a Barizilai, amene anadzitengera mkazi wa ana akazi a Barizilai Mgileadi, nachedwa ndi dzina lao.

64 Awa anafunafuna maina ao m'buku la iwo owerengedwa mwa cibadwidwe, koma osawapeza; potero anawayesa odetsedwa, nawacotsa ku nchito ya nsembe.

65 Ndipo kazembe anawauza kuti asadyeko zopatulikitsa, mpaka wauka wansembe wokhala ndi Urimu ndi Tumimu.

66 Msonkhano wonse pamodzi ndiwo zikwi makumi anai ndi ziwiri mphambu mazana atatu kudza makumi asanu ndi limodzi,

67 osawerenga akapolo ao amuna ndi akazi, ndiwo zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu mazana atatu ndi makumi atatu kudza asanu ndi awiri; ndipo anakhala nao amuna ndi akazi oyimbira mazana awiri mphambu makumi anai kudza asanu ndi mmodzi.

68 Akavalo ao ndiwo mazana asanu ndi awiri mphambu makumi atatu kudza asanu ndi mmodzi; nyuru zao mazana awiri mphambu makumi anai kudza zisanu

69 ngamira zao mazana anai mphambu makumi atatu kudza asanu aburu ao zikwi zisanu ndi cimodzi mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi awiri.

70 Ndipo ena a akuru a nyumba za makolo anapereka kunchito. Kazembeyo anapereka kucuma madariki agolidi cikwi cimodzi, mbale zawazira makumi asanu, maraya a ansembe makumi atatu.

71 Enanso a akuru a nyumba za makolo anapereka ku cuma ca nchitoyi, madariki agolidi zikwi makumi awiri, ndi miyeso ya siliva zikwi ziwiri mphambu mazana awiri.

72 Zopereka za anthu otsala ndizo madariki agolidi zikwi makumi awiri, ndi miyeso ya siliva zikwi ziwiri, ndi maraya a ansembe makumi asanu ndi limodzi mphambu asanu ndi awiri.

73 Nakhala m'midzi mwao ansembe, ndi Alevi, ndi odikira, ndi oyimbira, ndi anthu ena, ndi Anetini, ndi Aisrayeli onse. Utakhala tsono mwezi wacisanu ndi ciwiri ana a Israyeli anakhala m'midzi mwao.

8

1 Ndipo anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi ku khwalala liri ku cipata ca kumadzi, namuuza Ezara mlembi atenge buku la cilamulo ca Mose, cimene Yehova adalamulira Israyeli.

2 Ndipo Ezara wansembe anabwera naco cilamulo pamaso pa msonkhano, ndiwo amuna ndi akazi, ndi yense wakumva ndi kuzindikira tsiku loyamba la mwezi wacisanu ndi ciwiri.

3 Nawerenga m'menemo pa khwalala liri ku cipata ca kumadzi kuyambira mbanda kuca kufikira msana, pamaso pa amuna ndi akazi, ndi iwo okhoza kuzindikira; ndi anthu onse anacherera khutu buku la cilamulo.

4 Ndipo Ezara mlembi anaima pa ciunda ca mitengo adacimangira msonkhanowo; ndi pambali: pace padaima Matitiya, ndi Sema, ndi Anaya, ndi Uriya, ndi Hilikiya, ndi Maaseya, ku dzanja lamanja lace; ndi ku dzanja lamanzere Pedaya, ndi Misayeli, ndi Malikiya, ndi Hasumu, ndi Hasibadana, Zekariya, ndi Mesulamu.

5 Ndipo Ezara anafunyulula bukulo pamaso pa anthu onse, popeza iye anasomphokera anthu onse; ndipo polifunyulula anthu onse ananyamuka.

6 Pamenepo Ezara analemekeza Yehova Mulungu wamkuru. Nabvomereza anthu onse, ndi kuti, Amen, Amen; nakweza manja ao, nawerama, nalambira Yehova nkhope zao pansi.

7 Ndi Yesuwa, ndi Bani, ndi Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetai, Hodayi, Maaseya, Kelita, Azariya, Yozabadi, Hanani, Pelaya, ndi Alevi, anadziwitsa anthu cilamuloco; ndi anthu anali ciriri pamalo pao,

8 Nawerenga iwo m'buku m'cilamulo ca Mulungu momveka, natanthauzira, nawazindikiritsa cowerengedwaco.

9 Ndipo Nehemiya, ndiye kazembe, ndi Ezara wansembe mlembiyo, ndi Alevi ophunzitsa anthu, ananena ndi anthu onse, Lero ndilo lopatulikira Yehova Mulungu wanu, musamacita maliro, musamalira misozi. Popeza anthu onse analira misozi pakumva mau a cilamulo.

10 Nanena naonso, Mukani mukadye zonona, mukamwe zozuna, nimumtumizire gawo lace iye amene sanamkonze ratu kanthu; cifukwa lero ndilo lopatulikira Ambuye wathu; ndipo musamacita cisoni; pakuti cimwemwe ca Yehova ndico mphamvu yanu.

11 Ndipo Alevi anatontholetsa anthu onse, ndi kuti, Khalani muli cete; pakuti lero ndi lopatulika; musamacita cisoni.

12 Napita anthu onse kudya ndi kumwa, ndi kutumiza magawo, ndi kusekerera kwakukuru; popeza anazindikira mau amene adawafotokozera.

13 Ndipo m'mawa mwace akuru a nyumba za makolo a anthu onse, ansembe, ndi Alevi anasonkhana pamodzi kwa Ezara mlembi, kuti atole nzeru za mau a cilamulo.

14 Napeza munalembedwa m'cilamulo kuti Yehova analamulira ndi Mose, kuti ana a Israyeli azikhala m'misasa pa madyerero a mwezi wacisanu ndi ciwiri,

15 ndi kuti azilalikira ndi kumveketsa m'midzi mwao monse ndi m'Yerusalemu, ndi kuti, Muziturukira kuphiri, ndi kutengako nthambi za azitona, ndi nthambi za mitengo yamafuta, ndi nthambi za mitengo yamcisu, ndi zinkhwamba za migwalangwa, ndi nthambi za mitengo zothonana, kumanga nazo misasa monga munalembedwa.

16 Naturuka anthu, nakazitenga, nadzimangira misasa, yense pa tsindwi la nyumba yace, ndi m'mabwalo ao, ndi m'mabwalo a nyumba ya Mulungu, ndi pa khwalala la cipata ca kumadzi, ndi pa khwalala la cipata ca Efraimu.

17 Ndi msonkhano wonse wa iwo oturuka m'ndende anamanga misasa, nakhala m'misasamo; pakuti ciyambire masiku a Yesuwa mwana wa Nuni kufikira tsiku lija ana a Israyeli sanatero. Ndipo panali cimwemwe cacikuru.

18 Anawerenganso m'buku la cilamulo ca Mulungu tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba kufikira tsiku lotsiriza. Nacita madyerero masiku asanu ndi awiri; ndi tsiku lacisanu ndi citaru ndilo msonkhano woletsa, monga mwa malemba.

9

1 Ndipo tsiku la makumi awiri mphambu anai la mwezi uno ana a Israyeli anasonkhana ndi kusala, ndi kubvala ciguduli, ndipo anali ndi pfumbi.

2 Nadzipatula a mbumba ya Israyeli kwa alendo onse, naimirira, naulula zocimwa zao, ndi mphulupulu za makolo ao.

3 Naimima poima pao, nawerenga m'buku la cilamulo ca Yehova Mulungu wao limodzi la magawo anai a tsiku; ndi limodzi la magawo anai anaulula, napembedza Yehova Mulungu wao.

4 Pamenepo anaimirira pa ciunda ca Alevi Yesuwa, ndi Bani, Kadimiyeli, Sebaniya, Buni, Serebiya, Bani, ndi Kenani, napfuula ndi mau akuru kwa Yehova Mulungu wao.

5 Nati Alevi, Yesuwa, ndi Kadimiyeli, Buni, Hasabineya, Serebiya, Hodiya, Sebaniya, ndi Petatiya, Imirirani, lemekezani Yehova Mulungu wanu ku nthawi za nthawi; ndipo lilemekezeke dzina lanu la ulemerero, lokuzika loposa cilemekezo ndi ciyamiko conse.

6 Inu ndinu Yehova, nokhanu; mwalenga thambo, kumwambamwamba, ndi khamu lao lonse, dziko lapansi, ndi zonse ziri pomwepo, nyanja ndi zonse ziri m'mwemo, ndi Inu muzisunga zamoyo zonsezi, ndi khamu la kumwamba lilambira Inu.

7 Inu ndinu Yehova Mulungu amene munasankha Abramu ndi kumturutsa m'Uri wa Akasidi, ndi kumucha dzina lace Abrahamu;

8 ndipo munampeza mtima wace wokhulupirika pamaso panu, nimunapangana naye kumpatsa dziko la Akanani, Ahiti, Aamori, ndi Aperizi, ndi Ayebusi, ndi Agirigasi, kulipereka kwa mbumba zace; ndipo mwakwaniritsa mau anu, popeza Inu ndinu wolungama.

9 Ndipo munapenya msauko wa makolo athu m'Aigupto, nimunamva kupfuula kwao ku Nyanja Yofiira,

10 nimunacitira zizindikilo ndi zodabwiza Farao ndi akapolo ace onse, ndi anthu onse a m'dziko lace; popeza munadziwa kuti anawacitira modzikuza; ndipo munadzibukitsira dzina monga lero lino.

11 Ndipo munagawanitsa nyanja pamaso pao, napita iwo pakati pa nyanja pouma, ndipo munaponya mozama owalondola, ngati mwala m'madzi olimba.

12 Munawatsogoleranso usana ndi mtambo woti njo, ndi moto tolo usiku, kuwaunikira m'njira akayendamo.

13 Munatsikiranso pa phiri la Sinai, nimunalankhula nao mocokera m'Mwamba, ndipo munawapatsa maweruzo oyenera, ndi cilamulo coona, malemba, ndi malamulo okoma;

14 ndi Sabata lanu lopatulika munawadziwitsa, nimunawalamulira malamulo, ndi malemba, ndi cilamulo, mwa dzanja la Mose mtumiki wanu;

15 ndi mkate wocokera m'mwamba munawapatsa pa njala yao; ndi madzi oturuka m'thanthwe munawaturutsira pa ludzu lao, ndi kuwauza alowe, nalandire dziko limene mudakwezapo dzanja lanu kuwapatsa.

16 Koma iwo ndi makolo athu anacita modzikuza, naumitsa khosi lao, osamvera malamulo anu,

17 nakana kumvera, osakumbukilansozodabwiza zanu munazicita pakati pao; koma anaumitsa khosi lao, ndipo m'kupanduka kwao anaika mtsogoleri abwerere kumka ku ukapolo wao; koma Inu ndinu Mulungu wokhululukira, wacisomo, ndi wansoni, wolekereza, ndi wocuruka cifundo; ndipo simunawasiya.

18 Ngakhale apa atadzipangira mwana wa ng'ombe woyenga, nati, Suyu Mulungu wako anakukweza kucokera ku Aigupto, nacita zopeputsa zazikuru;

19 koma Inu mwa nsoni zanu zazikuru simunawasiya m'cipululu; mtambo woti njo sunawacokera usana kuwatsogolera m'njira, ngakhale moto wa tolo usiku kuwaunikira panjira anayenera kuyendamo.

20 Munawapatsanso mzimu wanu wokoma kuwalangiza, ndipo simunawamana mana anu pakamwa pao; munawapatsanso madzi pa ludzu lao.

21 Ndipo munawalera zaka makumi anai m'cipululu, osasowa kanthu iwo; zobvala zao sizinatha, ndi mapazi ao sanatupa.

22 Munawapatsanso maufumu, ndi mitundu ya anthu, nimunawagawa m'madera, motero analandira likhale lao lao dziko la Sihoni, ndilo dziko la mfumu ya ku Hesiboni, ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basana.

23 Ana aonso munawacurukitsa monga nyenyezi za m'mwamba, nimunawalowetsa m'dziko mudalinena kwa makolo ao, alowemo likhale lao lao.

24 Nalowa anawo, nalandira dzikoli likhale lao lao, ndipo munagonjetsa pamaso pao okhala m'dziko, ndiwo Akanani, ndi kuwapereka m'dzanja mwao, pamodzi ndi mafumu ao, ndi mitundu ya anthu ya m'dziko, kuti acite nao cifuniro cao.

25 Ndipo analanda midzi yamalinga, ndi dziko la zonona, nalandira zikhale zao zao nyumba zodza la ndi zokoma ziri zonse, zitsime zokumbidwa, minda yampesa, ndi minda yaazitona, ndi mitengo yambiri yazipatso; nadya iwo, nakhuta, nanenepa, nakondwera nako kukoma kwanu kwakukuru.

26 Koma anakhala osamvera, napandukira Inu, nataya cilamulo canu m'mbuyo mwao napha aneneri anu akuwacitira umboni, kuwabwezera kwa Inu, nacita zopeputsa zazikuru.

27 Cifukwa cace munawapereka m'dzanja la adani ao akuwasautsa; koma mu nthawi ya kusautsika kwao anapfuula kwa Inu, ndipo munamva m'Mwamba, ndi monga mwa nsoni zanu zambiri munawapatsa apulumutsi akuwapulumutsa m'dzanja la adani ao.

28 Koma atapumula, anabwereza kucita coipa pamaso panu; cifukwa cace munawasiya m'dzanja la adani ao amene anacita ufumu pa iwo; koma pobwera iwo ndi kupfuula kwa Inu, munamva m'Mwamba ndi kuwapulumutsa kawiri kawiri, monga mwa cifundo canu;

29 ndipo munawacitira umboni, kuti muwabwezerenso ku cilamulo canu; koma anacita modzikuza, osamvera malamulo anu; koma anacimwira malamulo anu (amene munthu akawacita adzakhala nao ndi moyo); nakaniza phewa lao, naumitsa khosi lao, osamvera.

30 Koma munawalekerera zaka zambiri, ndi kuwacitira umboni ndi mzimu wanu, mwa aneneri anu, koma sanamvera; cifukwa cace munawapereka m'dzanja la mitundu ya anthu a m'dziko.

31 Ndipo mwa nsoni zanu zocuruka simunawatha, kapena kuwataya; popeza Inu ndinu Mulungu wa cisomo ndi cifundo.

32 Ndipo tsono, Mulungu wathu, ndinu Mulungu wamkuru, ndi wamphamvu, ndi woopsa, wakusunga pangano ndi cifundo, asacepe pamaso panu mabvuto athu onse amene anatigwera ife, ndi mafumu athu, akuru athu, ndi ansembe athu, ndi aneneri athu, ndi makolo athu, ndi anthu anu onse, kuyambira masiku a mafumu a Asuri, mpaka lero lino.

33 Koma Inu ndinu wolungama mwa zonse zatigwera; pakuti mwacita zoona, koma ife tacita coipa;

34 ndi mafumu athu, akuru athu, ansembe athu, ndi makolo athu, sanasunga cilamulo canu, kapena kumvera malamulo anu, ndi mboni zanu, zimene munawacitira umboni nazo.

35 Popeza sanatumikira Inu m'ufumu wao, ndi m'ubwino wanu wocuruka umene mudawapatsa, ndi m'dziko lalikuru ndi la zonona mudalipereka pamaso pao, ndipo sanabwerera kuleka nchito zao zoipa.

36 Tapenyani, ife lero ndife akapolo, ndi dzikoli mudalipereka kwa makolo athu kudya zipatso zace ndi zokoma zace, taonani, ife ndife akapolo m'menemo.

37 Ndipo licurukitsira mafumu zipatso zace, ndiwo amene munawaika atiweruze, cifukwa ca zoipa zathu; acitanso ufumu pa matupi athu, ndi pa zaweta zathu, monga umo akonda; ndipo ife tisauka kwakukuru.

38 Ndipo mwa ici conse ticita pangano lokhazikika, ndi kulilemba, ndi akulu athu, Alevi athu, ndi ansembe athu, alikomera cizindikilo.

10

1 Okomera cizindikilo tsono ndiwo Nehemiya, Tirisata mwana wa Hakaliya, ndi Zedekiya,

2 Seraya, Agariya, Yeremiya,

3 Pasuri, Amariya, Malikiya,

4 Hatusi, Sebaniya, Maluki,

5 Harimu, Meremoti, Obadiya,

6 Danieli, Ginetoni, Baruki,

7 Mesulamu, Abiya, Miyamini,

8 Maaziya, Biligai, Semaya, ndiwo ansembe.

9 Ndi Alevi ndiwo Yesuwa mwana wa Azaniya, Binui wa ana a Henadadi, Kadiniyeli;

10 ndi abale ao: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,

11 Mika, Rehobo, Hasabiya,

12 Zakuri, Serebiya, Sebaniya,

13 Hodiya, Bani, Beninu.

14 Akuru a anthu: Parosi, Patati, Moabu, Elamu, Zatu, Bani,

15 Buni, Azigadi, Bebai,

16 Adoniya, Bigivai, Adini,

17 Ateri, Hezekiya, Azuri,

18 Hodiya, Hasumu, Bezai,

19 Harifi, Anatoti, Nobai,

20 Magipiasi, Mesulamu, Heziri,

21 Mesezabele, Zadoki, Yaduwa,

22 Pelatiya, Hanani, Ananiya,

23 Hoseya, Hananiya, Hasubi,

24 Halohesi, Pila, Sobeki,

25 Rehumu, Hasabina, Maaseya,

26 ndi Ahiya, Hanani, Anani,

27 Maluki, Harimu, Baana.

28 Ndi anthu otsala, ansembe, Alevi, odikira, oyimbira, Anetini, ndi onse anadzisiyanitsawo pa mitundu ya anthu a m'dziko kutsata cilamulo ca Mulugu, akazi ao, ana ao amuna ndi akazi, yense wodziwa ndi wozindikira,

29 amenewa anaumirira abale ao, omveka ao, nalowa m'temberero ndi lumbiro, kuti adzayenda m'cilamulo ca Mulungu anacipereka Mose mtumiki wa Mulungu, ndi kuti adzasunga ndi kucita zonse atilamulira Yehova Ambuye wathu, ndi maweruzo ace, ndi malemba ace;

30 ndi kuti sitidzapereka ana athu akazi kwa mitundu ya anthu a m'dziko, kapena kutengera ana athu amuna ana ao akazi;

31 ndipo mitundu ya anthu a m'dziko akabwera nao malonda, ngakhale tirigu, dzuwa la Sabata, kutsata malonda, sitidzagulana nao dzuwa la Sabata, kapena dzuwa lina lopatulika, ndi kuti tidzaleka caka cacisanu ndi ciwiri ndi mangawa ali onse.

32 Tinadziikiranso malamulo, kuti tizipereka caka ndi caka limodzi la magawo atatu a sekeli ku nchito ya nyumba ya Mulungu wathu;

33 kuliperekera mkate woonekera, ndi nsembe yaufa yosaleka, ndi nsembe yopsereza yosaleka, ya masabata, ya pokhala miyezi, kuliperekera nyengo zoikika ndi zopatulikira, ndi nsembe za zolakwa za kutetezera Israyeli zoipa, ndi nchito zonse za nyumba ya Mulungu wathu.

34 Ndipo tinalota maere, ansembe, Alevi, ndi anthu, a copereka ca nkhuni, kubwera nazo ku nyumba ya Mulungu wathu, monga mwa nyumba za makolo athu, pa nyengo zoikika caka ndi caka, kuzisonkha pa guwa la nsembe la Yehova Mulungu wathu, monga mulembedwa m'cilamulo;

35 ndi kubwera nazo zipatso zoyamba za nthaka, ndi zoyamba za zipatso zonse za mtengo uli wonse caka ndi caka, ku nyumba ya Yehova;

36 ndi ana athu oyamba kubadwa, ndi oyamba kubadwa a nyama zathu, monga mulembedwa m'cilamulo, ndi oyamba a ng'ombe zathu, ndi nkhosa zathu, kubwera nazo ku nyumba ya Mulungu wathu kwa ansembe akutumikira m'nyumba ya Mulungu wathu;

37 ndi kuti tidzabwera nazo za mtanda wa mkate wathu woyamba, ndi nsembe zathu zokwera, ndi zipatso za mtengo uli wonse, vinyo, ndi mafuta, kwa ansembe, ku zipinda za nyumba ya Mulungu wathu; ndi limodzi la magawo khumi la nthaka yathu kwa Alevi; pakuti Alevi amene amalandira limodzi limodzi la magawo khumi m'midzi yonse yolima ife.

38 Ndipo wansembe mwana wa Aroni azikhala ndi Alevi, polandira Alevi limodzi limodzi la magawo khumi; ndi Alevi azikwera nalo limodzi la magawo khumi mwa limodzi limodzi la magawo khumi ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda, ku nyumba ya cuma.

39 Pakuti ana a Israyeli ndi ana a Levi, azibwera nayo nsembe yokweza yatirigu, ndi yavinyo ndi yamafuta, kuzipinda kuli zipangizo za malo opatulika, ndi ansembe akutumikira, ndi odikira, ndi oyimbira; kuti tisasiye nyumba ya Mulungu wathu.

11

1 Ndipo akuru anthu anakhala m'Yerusalemu; anthu otsala omwe anacita maere, kuti libwere limodzi la magawo khumi likhale m'Yerusalemu, mudzi wopatulika, ndi asanu ndi anai a khumi m'midzi yina.

2 Ndipo anthu anadalitsa amuna onse a akudzinenera mwaufulu kuti adzakhala m'Yerusalemu.

3 Awa tsono ndi akulu a dziko okhala m'Yerusalemu; koma m'midzi ya Yuda yense anakhala pa colowa cace m'midzi mwao, ndiwo Israyeli, ansembe, ndi Alevi, ndi Anetini, ndi ana a akapolo a Solomo.

4 Ndipo m'Yerusalemu munakhala ena a ana a Yuda ndi a ana a Benjamini. Mwa ana a Yuda: Ataya mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya, mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli, wa ana a Perezi;

5 ndi Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koloze, mwana wa Huzaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yoyaribi, mwana wa Zekariya, mwana wa Msiloni.

6 Ana onse a Perezi okhala m'Yerusalemu ndiwo ngwazi mazana anai mphambu makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi atatu.

7 Ndi ana a Benjamini ndi awa: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yoedi, mwana wa Pedaya, mwana Wa Kolaya, mwana wa Maseya, mwana wa Itiyeli, mwana wa Yesaya.

8 Ndi wotsatananaye Gabai, Salai, mazana asanu ndi anai mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.

9 Ndi Yoeli mwana wa Zikiri ndiye woyang'anira wao, ndi Yuda mwana wa Hasenuwa ndiye wothandizana naye, poyang'anira mudzi.

10 Mwa ansembe: Yedaya mwana wa Yoyaribi, Yakini,

11 Seraya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubu mtsogoleri wa m'nyumba ya Mulungu;

12 ndi abale ao ocita nchito ya m'nyumbayi ndiwo mazana asanu ndi atatu mphambu makumi awiri kudza awiri; ndi Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amzi, mwana wa Zekariya, mwana: wa Pasuru, mwana wa Malikiya;

13 ndi abale ace akulu a nyumba za makolo awiri mphambu makumi anai kudza awiri, ndi Amasai mwana wa Azareli, mwana wa Azai, mwana wa Mesilimoti, mwana wa Imeri;

14 ndi abale ao, ngwazi zamphamvu, zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu; ndi woyang'anira wao ndiye Zabidiyeli mwana wa Hagedolimu.

15 Ndi mwa Alevi: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni;

16 ndi Sabetai, ndi Yozabadi, mwa akuru a Alevi, anayang'anira nchito za pabwalo za nyumba ya Mulungu;

17 ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu, ndiye mkuru wakuyamba mayamiko, popemphera; ndi Bakibukiya wotsatana naye mwa abale ace, ndi Abida mwana wa Samua, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.

18 Alevi onse m'mudzi wopatulikawo ndiwo mazana awiri mphambu makumi asanu ndi atatu kudza anai.

19 Ndi odikira: Akubu, Talimoni, ndi abale ao akulindira pazipata, ndiwo zana limodzi mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.

20 Ndi Aisrayeli otsala, ndiwo ansembe ndi Alevi, anakhala m'midzi yonse ya Yuda, yense m'colowa cace.

21 Koma Anetini anakhala m'Ofeli, ndi Ziya, ndi Gisipa anali oyang'anira Anetini.

22 Ndipo woyang'anira wa Alevi m'Yerusalemu ndiye Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika; mwa ana a Asafu oyimbira ena anayang'anira nchito ya m'nyumba ya Mulungu.

23 Pakuti mfumu inalamulira za iwowa, naikira oyimbira cowathandiza, yense cace pa tsiku lace.

24 Ndi Petatiya mwana wa Mesezabele, wa ana a Zera, mwana wa Yuda, anatumikira mfumu pa mirandu yonse ya anthuwo.

25 Ndi ana ena a Yuda anakhala m'midzi ya ku minda yao, m'Kiriyati Ariba ndi miraga yace, ndi m'Diboni ndi miraga yace, ndi m'Yekabizeeli ndi midzi yace,

26 ndi m'Yesuwa, ndi m'Molada, ndi Betepeleti,

27 ndi m'Hazarisuala, ndi m'Beereseba ndi miraga yace,

28 ndi m'Zikilaga, ndi m'Mekona ndi miraga yace,

29 ndi m'Enirimoni, ndi m'Zora, ndi m'Yarimuti,

30 Zanowa, Adulamu ndi midzi yao, Lakisi ndi minda yace, Azeka ndi miraga yace. Ndipo anamanga misasa kuyambira ku Beereseba mpaka cigwa ca Hinomu.

31 Ana a Benjamini omwe, kuyambira ku Geba pa Mikimasi, ndi Aiya, ndi pa Beteli ndi miraga yace,

32 pa Anatoti, Nobi, Ananiya,

33 Hazori, Rama, Gitaimu,

34 Hadidi, Zeboimu, Nebalati,

35 Lodi, ndi Ono, cigwa ca amisiri.

36 Ndi magawo a Levi anakhala ena ku Yuda, ndi ena ku Benjamini.

12

1 Ndipo ansembe ndi Alevi amene anakwera ndi Zerubabele mwana wa Sealtiyeli, ndi Yesuwa, ndi awa: Seraya, Yeremiya, Ezara,

2 Amariya, Maluki, Hatusi,

3 Sekaniya, Rehumu, Meremoti,

4 Ido, Ginetoi, Abiya,

5 Miyamini, Maadiya, Biliga,

6 Semaya, ndi Yoyaribi, Yedaya,

7 Salu, Amoki, Hilikiya, Yedaya. Awa ndi akuru a ansembe ndi abale ao m'masiku a Yesuwa.

8 Ndi Alevi ndiwo Yesuwa, Binui, Kadimiyeli, Serebiya, Yuda, ndi Mataniya; iye ndi abale ace amatsogolera mayamiko.

9 Ndi Bakibukiya ndi Uni, abale ao, anawayang'anira maulonda.

10 Ndi Yesuwa anabala Yoyakimu, ndi Yoyakimu anabala Eliasibi ndi Eliasibi anabala Yoyada,

11 ndi Yoyada anabala Yonatani, ndi Yonatani, anabala Yaduwa.

12 Ndi m'masiku a Yoyakimu ansembe akulu a nyumba za makolo ndiwo: wa Seraya, Meraya; wa Yeremiya, Hananiya;

13 wa Ezara, Mesulamu; wa Amariya, Yehohanana;

14 wa Maluki, Yonatani; wa Sebaniya, Yosefe;

15 wa Harimu, Adina; wa Merayoti, Helikai;

16 wa Ido, Zekariya; wa Ginetoni, Mesulamu;

17 wa Abiya, Zikiri; wa Minyamini, wa Moadiya, Pilitai;

18 wa Biliga, Samura; wa Semaya, Yehonatani;

19 ndi wa Yoyaribi, Matani; wa Yedaya, Uzi;

20 wa Salai, Kalai; wa Amoki, Eberi;

21 wa Hilikiya, Hasabiya; wa Yedaya, Netaneli.

22 M'masiku a Ehasibi, Yoyada, Yohanana, ndi Yoduwa, Alevi analembedwa akuru a nyumba za makolo; ansembe omwe, mpaka ufumu wa Dariyo wa ku Perisiya.

23 Ana a Levi, akuru a nyumba za makolo, analembedwa m'buku la macitidwe, mpaka masiku a Yohanana mwana wa Eliasibu.

24 Ndi akuru a Alevi: Hasabiya, Serebiya, ndi Yesuwa mwana wa Kadimiyeli, ndi abale ao openyana nao, kulemekeza ndi kuyamika, monga mwa lamulo la Davide munthu wa Mulungu, alonda kupenyana alonda.

25 Mataniya, ndi Bakibukiya, Obadiya, Mesulamu, Talimoni, Akubi, ndiwo odikira akulonda pa nyumba za cuma ziri kuzipata.

26 Awa anakhala m'masiku a Yoyakimu mwana wa Yesuwa, mwana wa Yozadaki, ndi m'masiku a Nehemiya kazembe, ndi a Ezara wansembe mlembiyo.

27 Ndipo popereka linga la Yerusalemu anafunafuna Alevi m'malo mwao monse, kubwera nao ku Yerusalemu, kuti acite kuperekaku mokondwera, ndi mayamiko, ndi kuyimbira, ndi nsanje, zisakasa, ndi azeze.

28 Ana a oyimbirawo anasonkhana ocokera ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku midzi ya Anetofati,

29 ndi ku Betegiligala, ndi ku minda ya Geba ndi Azimaveti; popeza oyimbirawo adadzimangira midzi pozungulira Yerusalemu.

30 Ndipo ansembe ndi Alevi anadziyeretsa okha, nayeretsa anthu, ndi zipata, ndi linga.

31 Pamenepo ndinakwera nao akuru a Yuda pa lingali, ndinaikanso oyamikira magulu awiri akuru oyenda molongosoka; lina loyenda ku dzanja lamanja palinga kumka ku cipata ca kudzala;

32 ndi pambuyo pao anayenda Hosaya, ndi limodzi la magawo awiri a akuru a Yuda,

33 ndi Azariya, Ezara ndi Mesulamu,

34 Yuda, ndi Benjamini, ndi Semaya, ndi Yeremiya,

35 ndi ana ena a ansembe ndi malipenga: Zekariya mwana wa Yonatani, mwana wa Semaya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mikaya, mwana wa Zakuri, mwana wa Asafu,

36 ndi abale ace: Semaya, ndi Azareli, Milalai, Gilelai, Maai, Netaneli, ndi Yuda, Hanani, ndi zoyimbira za Davide munthu wa Mulungu; ndi Ezara mlembiyo anawatsogolera;

37 ndi ku cipata ca kucitsime, ndi kundunji kwao, anakwerera pa makwerero a mudzi wa Davide, potundumuka linga, popitirira pa nyumba ya Davide, mpaka ku cipata ca kumadzi kum'mawa.

38 Ndi gulu lina la oyamikira linamuka mokomana nao, ndi ine ndinawatsata, pamodzi ndi limodzi la magawo awiri la anthu palinga, napitirira pa nsanja ya ng'anjo, mpaka ku linga lacitando;

39 ndi pamwamba pa cipata ca Efraimu, ndi ku cipata cakale, ndi ku cipata cansomba, ndi nsanja ya Hananeli, ndi nsanja ya Hameya, mpaka ku cipata cankhosa; ndipo anaima ku cipata cakaidi.

40 Atatero, magulu awiriwo a iwo oyamikira anaima m'nyumba ya Mulungu, ndipo ine ndi limodzi la magawo awiri a olamulira pamodzi ndi ine;

41 ndi ansembe, Eliakimu, Maaseya, Minyamini, Mikaya, Elioenai, Zekariya, ndi Hananiya, ali nao malipenga;

42 ndi Maaseya, ndi Semaya, ndi Eleazara, ndi Uzi, ndi Yehohanana, ndi Malikiya, ndi Elamu, ndi Ezeri. Ndipo oyimbira anayimbitsa Yeziraya ndiye woyang'anira wao.

43 Ndipo anaphera nsembe zambiri tsiku lija, nasekerera; pakuti Mulungu anawakondweretsa ndi cimwemwe cacikuru; ndi akazi omwe ndi ana anakondwera; ndi cikondwerero ca Yerusalemu cinamveka kutali.

44 Ndipo tsiku lomwelo anaika anthu asunge zipinda za cuma, za nsembe zokweza, za zipatso zoyamba, ndi za limodzi limodzi la magawo khumi, kulonga m'mwemo, monga mwa minda ya midzi, magawo onenedwa ndi cilamulo, akhale a ansembe ndi Alevi; popeza Yuda anakondwera nao ansembe ndi Alevi lakuimirirako.

45 Ndipo iwo anasunga udikiro wa Mulungu wao, ndi udikiro wa mayeretsedwe; momwemonso oyimbira ndi odikira, monga mwa lamulo la Davide ndi la Solomo mwana wace.

46 Pakuti m'masiku a Davide ndi Asafu kalelo kunali mkuru wa oyimbira, ndi wa nyimbo zolemekeza ndi zoyamikira Mulungu.

47 Ndi Aisrayeli onse m'masiku a Zerubabele, ndi m'masiku a Nehemiya, anapereka magawo a oyimbira ndi odikira, monga mudafunika tsiku ndi tsiku; nawapatulira Alevi; ndi Alevi anawapatulira ana a Aroni.

13

1 Tsiku lomwelo anawerenga m'buku la Mose m'makutu a anthu, napeza m'menemo kuti Aamoni ndi Amoabu asalowe mu msonkhano wa Mulungu ku nthawi yonse;

2 popeza sanawacingamira ana a Israyeli ndi cakudya ndi madzi, koma anawalemberera Balamu awatemberere; koma Mulungu wathu anasanduliza tembererolo likhale mdalitso.

3 Ndipo kunali, atamva cilamuloco, anasiyanitsa pa Israyeli anthu osokonezeka onse.

4 Cinkana ici, Eliasibu wansembe, woikidwa asunge zipinda za nyumba ya Mulungu wathu, anacita cibale ndi Tobiya,

5 namkonzera cipinda cacikuru, kumene adasungira kale zopereka za ufa, libano, ndi zipangizo, ndi limodzi limodzi la magawo khumi a tirigu, vinyo, ndi mafuta, zolamutidwira Alevi, ndi oyimbira, ndi odikira, ndi nsembe zokweza za ansembe.

6 Koma pocitika ici conse sindinakhala ku Yerusalemu; pakuti caka ca makumi atatu ndi caciwiri ca Aritasasta mfumu ya Babulo ndinafika kwa mfumu, ndipo atapita masiku ena ndinapempha mfumu indilole;

7 ndipo ndinafika ku Yerusalemu, ndi kuzindikira coipa anacicita Eliasibu, cifukwa ca Tobiya, ndi kumkonzera cipinda m'mabwalo a nyumba ya Mulungu.

8 Ndipo ndinaipidwa naco kwambiri, motero ndinataya kubwalo akatundu onse a m'nyumba ya Tobiya, kuwacotsa m'cipindamo.

9 Pamenepo ndinalamulira, ndipo anayeretsa zipindazo; ndipo ndinabwezeramonso zipangizo za nyumba ya Mulungu, pamodzi ndi zopereka za ufa ndi libano.

10 Ndinazindikiranso kuti sanapereka kwa Alevi magawo ao; m'mwemo Alevi ndi oyimbira adathawira yense ku munda wace.

11 Potero ndinatsutsana nao olamulira, ndinati, Yasiyidwiranji nyumba ya Mulungu? Ndipo ndinawasonkhanitsa, ndi kuwafka m'malo mwao.

12 Ndi Ayuda onse anabwera nalo limodzi limodzi la magawo khumi a tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta, ku nyumba za cuma.

13 Ndinaikanso osunga cuma, asunge nyumba za cuma: Selemiya wansembe, ndi Zadoki mlembi; ndi wa Alevi, Pedaya; ndi wakuwathandiza, Hanani mwana wa Zakuri, mwana wa Mataniya; popeza anayesedwa okhulupirika ndi udindo wao, ndiwo kugawira abale ao.

14 Mundikumbukile Mulungu wanga mwa ici, nimusafafanize zokoma zanga ndinazicitira nyumba ya Mulungu wanga, ndi maudikiro ace.

15 Masiku awa ndinaona ku Yuda ena akuponda mphesa m'coponderamo dzuwa la Sabata, ndi akubwera nayo mitolo ya tirigu, ndi kuisenzetsa pa aburu; momwemonso vinyo, mphesa, ndi nkhuyu, ndi zosenza ziri zonse, zimene analowa nazo m'Yerusalemu dzuwa la Sabata, ndipo ndinawacitira umboni wakuwatsutsa tsikuti anagulitsa zakudya.

16 Anakhalanso m'menemo a ku Turo, obwera nazo nsomba, ndi malonda ali onse, nagulitsa dzuwa la Sabata kwa ana a Yuda ndi m'Yerusalemu.

17 Pamenepo ndinatsutsana nao aufulu a Yuda, ndinanena nao, Cinthu canji coipa ici mucicita, ndi kuipsa naco dzuwa la Sabata?

18 Sanatero kodi makolo anu, ndipo Mulungu wathu anatifikitsira ife ndi mudzi uno coipa ici conse? koma inu muonjezera Israyeli mkwiyo pakuipsa Sabata.

19 Ndipo kunali, kukadayamba cizirezire pa zipata za Yerusalemu, losafika Sabata, ndinawauza atseke pamakomo; ndinawauzanso kuti asatsegulepo, koma litapita Sabata ndipo; ndipo ndinaimika anyamata anga ena pazipata, kuti pasalowe katundu dzuwa la Sabata.

20 Momwemo eni malonda ndi ogulitsa malonda ali onse, anagona kunja kwa Yerusalemu kamodzi kapena kawiri.

21 Koma ndinawacima umboni wakuwatsutsa, ndinanena nao, Mugoneranji pafupi pa linga? mukateronso ndikuthirani manja. Kuyambira pomwepo sanafikanso pa Sabata.

22 Ndipo ndinauza Alevi kuti adziyeretse, nabwere, nasunge pazipata kupatula dzuwa la Sabata. Mundikumbukire Icinso, Mulungu wanga, ndi kundileka monga mwa cifundo canu cacikuru.

23 Masiku aja ndinaonanso Ayudawo anadzitengera akazi a Asidodi, Aamoni, ndi Amoabu,

24 ndi ana ao analankhula mwina Ciasidodi, osadziwitsa kulankhula Ciyuda, koma monga umo amalankhula mtundu wao uli wonse.

25 Ndipo ndinatsutsana nao, ndi kuwatemberera, ndi kukantha ena a iwo, ndi kumwetula tsitsi lao, ndi kuwalumbiritsa pa Mulungu ndi kuti, Musapereka ana anu akazi kwa ana ao amuna, kapena kutengera ana anu amuna, kapena a inu nokha, ana ao akazi.

26 Nanga Solomo mfumu ya Israyeli sanacimwa nazo zinthu izi? cinkana mwa amitundu ambiri panalibe mfumu ngati iye, ndi Mulungu wace anamkonda, ndi Mulungu wace anamlonga mfumu ya Aisrayeli onse; koma ngakhale iye, akazi acilendo anamcimwitsa.

27 Ndipo kodi tidzamvera inu, kucita coipa ici cacikuru conse, kulakwira Mulungu wathu ndi kudzitengera akazi acilendo?

28 Koma wina wa ana a Yoyada, mwana wa Eliasibu mkuru wa ansembe, anali mkamwini wa Sanibalati Mhoroni; cifukwa cace ndinampitikitsa kumcotsa kwa ine.

29 Muwakumbukile Mulungu wanga, popeza anadetsa unsembe, ndi pangano la unsembe, ndi la Alevi.

30 Momwemo ndinawayeretsa kuwacotsera acilendo onse, ndi kuikira udikiro ansembe ndi Alevi, yense ku nchito yace;

31 ndi copereka ca nkhuni pa nthawi zoikika, ndi wa zipatso zoyamba. Mundikumbukile, Mulungu wanga, cindikomere.