1 NDIPO panali munthu wina wa ku Ramatayimu Zofimu, wa dziko la mapiri la Efraimu, dzina lace ndiye Elikana, mwana wace wa Yerohamu, mwana wa Elihu, mwana wa Tohu, mwana wa Zufu, M-efraimu.
2 Iyeyu anali nao akazi awiri; winayo dzina lace ndi Hana, mnzace dzina lace ndi Penina. Ndipo Penina anaona ana, koma Hana anali wouma.
3 Ndipo munthuyu akakwera caka ndi caka kuturuka m'mudzi mwace kukalambira ndi kupereka nsembe kwa Mulungu wa makamu m'Silo. Ndipo pomwepo panali ana amuna awiri a Eli, ansembe a Yehova, ndiwo Hofeni ndi Pinehasi.
4 Ndipo pofika tsiku lakuti Elikana akapereka nsembe, iye anapatsa Penina mkazi wace, ndi ana ace onse, amuna ndi akazi, gawo lao;
5 koma anapatsa Hana magawo awiri, cifukwa anakonda Hana, koma Mulungu anatseka mimba yace.
6 Ndipo womnyodolayo anamputa kwakukuru, kuti amuwawitse mtima, popeza Yehova anatseka mimba yace.
7 Ndipo popeza munthuyo adatero caka ndi caka, popita mkaziyo ku nyumba ya Yehova, mnzaceyo amamputa; cifukwa cace iye analira misozi, nakana kudya.
8 Ndipo mwamuna wace Elikana anati kwa iye, Hana, umaliriranji? ndipo umakaniranji kudya? ndipo mtima wako uwawa ninji? Ine sindiri wakuposa ana khumi kwa iwe kodi?
9 Comweco Hana anauka atadya m'Silo, ndi kumwa. Ndipo Eli wansembeyo anakhala pa mpando wace pa mphuthu ya Kacisi wa Yehova.
10 Ndipo mkaziyo anali ndi mtima wowawa, napemphera kwa Yehova, naliratu misozi;
11 nalonjeza cowinda, nati, Yehova wa makamu, mukapenyera ndithu kusauka kwa mdzakazi wanu, ndi kukumbukila ine, ndi kusaiwala mdzakazi wanu, mukapatsa mdzakazi wanu mwana wamwamuna, ine ndidzampereka kwa Yehova masiku onse a moyo wace, ndipo palibe lumo lidzapita pamutu pace.
12 Ndipo panali, m'mene iye analikupempherabe pamaso pa Yehova, Eli anapenyerera pakamwa pace.
13 Koma Hana ananena mu mtima; milomo yace inatukula, koma mau ace sanamveka; cifukwa cace Eli anamuyesa woledzera.
14 Ndipo Eli anati kwa iye, Udzaleka liti kuledzera? cotsa vinyo wako.
15 Ndipo Hana anayankha, nati, Iai, mbuyanga. Ine ndiri mkazi wa mtima wacisoni; sindinamwa vinyo kapena cakumwa cowawa, koma ndinatsanulira mtima wanga pamaso pa Yehova.
16 Musamandiyesa mdzakazi wanu mkazi woipa; cifukwa kufikira lero ndinalankhula mwa kucuruka kwa kudandaula kwanga ndi kubvutika kwanga.
17 Pamenepo Eli anayankha nati, Pita ndi mtendere; ndipo Mulungu wa Israyeli akupatse copempha cako unacipempha, kwa iye.
18 Ndipo iye anati, Mumkomere mtima mdzakazi wanu. Comweco mkaziyo anamuka, nakadya, ndi nkhope yace siinakhalanso yacisoni.
19 Ndipo iwo anauka mamawa, nalambira pamaso pa Yehova, nabwerera, nafikanso kwao ku Rama; ndipo Elikana anadziwa mkazi wace Hana, Yehova namkumbukila iye.
20 Ndipo panali pamene nthawi yace inafika, Hana anaima, nabala mwana wamwamuna: namucha dzina lace Samueli, nati, Cifukwa ndinampempha kwa Yehova,
21 Ndipo munthuyo Elikana, ndi a pa banja lace onse, anakwera kukapereka kwa Yehova nsembe ya caka ndi caka, ndi ya cowinda cace.
22 Koma Hana sadakwera, cifukwa kuti anati kwa mwamuna wace, Sindidzakwerako kufikira mwanayo ataleka kuyamwa, pamenepo ndidzapita naye kuti aoneke pamaso pa Yehova, ndi kukhalako cikhalire.
23 Ndipo Elikana mwamuna wace anati, Cita cimene cikukomera nukhale kufikira utamletsa kuyamwa; komatu Yehova akhazikitse mau ace. Comweco mkaziyo anakhala nayamwitsa mwana wace, kufikira anamletsa kuyamwa.
24 Ndipo atamletsa kuyamwa anakwera naye, pamodzi ndi ng'ombe ya zaka zitatu, ndi efa wa ufa, ndi thumba la vinyo, nafika naye ku nyumba ya Yehova ku Silo; koma mwanayo anali wamng'ono.
25 Ndipo iwo anapha ng'ombe, nabwera naye mwanayo kwa Eli.
26 Ndipo mkaziyo ananena, Mbuye wanga, pali moyo wanu, zoonadi ine ndine mkazi uja ndidaima pano ndi inu, ndi kupemphera kwa Yehova.
27 Ndinampempha mwanayu; ndipo Yehova anandipatsa copemphacanga ndinacipempha kwa iye;
28 cifukwa cace inenso ndinampereka kwa Yehova; masiku onse a moyo wace aperekedwa kwa Yehova. Ndipo analambira Yehova pomwepo.
1 Ndipo Hana anapemphera, nati Mtima wanga umyuka mokondwera kwa Yehova, Nyanga yanga yakwezeka mwa Yehova; Pakamwa panga pakula kwa adani anga; Popeza ndikondwera m'cipulumutsocanu.
2 Palibe wina woyera ngati Yehova; Palibe wina koma Inu nokha; Palibenso thanthwe longa Mulungu wathu.
3 Musalankhulenso modzikuza kwambiri motero; M'kamwa mwanu musaturuke zolulutsa; Cifukwa Yehova ali Mulungu wanzeru, Ndipo iye ayesa zocita anthu.
4 Mauta a amphamvu anathyoka, Koma okhumudwawo amangiridwa ndi mphamvu m'cuuno.
5 Amene anakhuta anakasuma cakudya; Koma anjalawo anacira; Inde cumba cabala asanu ndi awiri: Ndipo iye amene ali ndi ana ambiri acita liwondewonde.
6 Yehova amapha, napatsa moyo: Iye amatsitsa kumanda, naukitsanso.
7 Yehova asaukitsa, nalemeza; Acepetsa, nakuzanso.
8 Amuutsa waumphawi m'pfumbi, Nanyamula wosowa padzala, Kukamkhalitsa kwa akalonga; Ndi kuti akhale naco colowa ca cimpando ca ulemerero; Cifukwa nsanamira za dziko lapansi nza Yehova, Ndipo iye anakhazika dziko pa izo,
9 Adzasunga mapazi a okoodedwaace, Koma oipawo adzawakhalitsa cete mumdima; Pakuti palibe munthu adzapambana ndi mphamvu,
10 Otsutsana ndi Yehova adzaphwanyika; Kumwamba iye adzagunda pa iwo: Yehova adzaweruza malekezero a dziko: Ndipo adzapatsa mphamvu mfumuyace, Nadzakweza nyanga ya wodzozedwa wace.
11 Ndipo Elikana anauka kwao ku Rama, mwanayo natumikira Yehova pamaso pa Eli wansembeyo.
12 Koma ana a Eli anali oipa; sanadziwa Yehova.
13 Ndipo macitidwe a ansembe akucitira anthu ndiwo, kuti pamene munthu ali yense akapereka nsembe, mnyamata wa wansembeyo akabwera, nyama iri ciwirire, ndi cobvuulira ca ngowe ca mana atatu m'dzanja lace;
14 nacipisa m'cimphuli, kapena mumkhate, kapena m'nkhali, kapena mumphika; yonse imene cobvuuliraco cinaiturutsa, wansembeyo anaitenga ikhale yace. Adafotero ku Silo ndi Aisrayeli onse akufika kumeneko.
15 Ngakhale asanayambe kupsereza mafuta, amadza mnyamata wa wansembe, namuuza wopereka nsembe, nati, Umpatse wansembeyo nyama yoti akaoce; pakuti safuna nyama yako yophika koma yaiwisi.
16 Ndipo ngati munthu akanena naye, Koma adzatentha mafuta tsopano apa, atatha, utenge monga mtima wako ufuna; uyo akanena naye, lai, koma undipatsire iyo tsopanoli, ukapanda kutero ndidzailanda.
17 Ndipo zoipa za anyamatawo zinali zazikuru ndithu pamaso pa Yehova; pakuti anthu anaipidwa ndi nsembe ya Yehova.
18 Koma Samueli anatumikira pamaso pa Yehova akali mwana, atamangira m'cuuno ndi efodi wabafuta.
19 Ndiponso amace akamsokera mwinjiro waung'ono, nabwera nao kwa iye caka ndi caka, pakudza pamodzi ndi mwamuna wace kudzapereka nsembe ya pacaka.
20 Ndipo Eli anadalitsa Elikana ndi mkazi wace, nati, Yehova akupatse mbeu ndi mkazi uyu m'malo mwa iye amene munampempha kwa Yehova. Ndipo iwowa anabwera kwao.
21 Ndipo Yehova anakumbukila Hana, naima iye, nabala ana amuna atatu, ndi ana akazi awiri. Ndipo mwanayo Samueli anakula pamaso pa Yehova.
22 Ndipo Eli anali wokalamba ndithu; namva zonse ana ace anacitira Aisrayeli onse, ndi kuti anagona ndi akazi akusonkhana pa khomo la cihema cokomanako.
23 Ndipo iye ananena nao, Mumacitiranji zotere? popeza ndirinkumva za macitidwe anu oipa kwa anthu onsewa.
24 Iai, ana anga, popeza mbiri imene ndirikuimva siri yabwino iai; mulikulakwitsa anthu a Yehova.
25 Munthu akacimwira munthu mnzace oweruza adzaweruza mrandu wace; koma ngati munthu acimwira Yehova, adzampembedzera ndani? Koma ngakhale adatero, iwo aja anakhalabe osamvera mau a atate wao, cifukwa Yehova adati adzawaononga.
26 Ndipo mwanayo Samueli anakulakula, ndipo Yehova ndi anthu omwe anamkomera mtima.
27 Ndipo anafika kwa Eli munthu wa Mulungu, nanena naye, Atero Yehova, Kodi Ine ndinadziulula kwa banja la kholo lako, muja anali m'Aigupto, m'nyumba ya Farao?
28 Kodi sindinasankhula iye pakati pa mafuko onse a Israyeli, akhale wansembe wanga, kuti apereke nsembe pa guwa langa, nafukize zonunkhira, nabvale efodi pamaso panga? Kodi sindinapatsa banja la kholo lako zopereka zonse za kumoto za ana a Israyeli?
29 Nanga umaponnderezeranji nsembe yanga ndi copereka canga, zimene ndinalamulira m'mokhalamo mwanga; ndipo ucitira ana ako ulemu koposa Ine, kudzinenepetsa inu nokha ndi zokometsetsa za zopereka zao zonse za Aisrayeli, anthu anga?
30 Cifukwa cace Yehova Mulungu wa Israyeli akuti, Ndinaterodi kuti banja lako ndi banja la kholo lako lidzayenda pamaso panga nthawi zonse; koma tsopano Yehova ati, Cikhale kutali ndi Ine; popeza amene andilemekeza Ine, Inenso ndidzawalemekeza iwowa, ndipo akundipeputsa Ine, adzapeputsidwa.
31 Ona, masiku alinkudza amene ndidzadula dzanja lako, ndi dzanja la nyumba ya kholo lako, kuti m'banja lako musakhalenso nkhalamba,
32 Ndipo udzaona masautso a mokhalamo Mulungu, m'malo mwa zabwino zonse iye akadacitira Israyeli. Banja lako lidzakhala opanda nkhalamba cikhalire.
33 Ndipo munthu wako, amene ndidzamleka osamlikha pa guwa langa, adzatha maso ako, ndi kumvetsa mtima wako cisoni; ndipo obadwa onse a m'banja lako adzamwalira akali biriwiri.
34 Ndipo ici cimene cidzafikira ana ako awiri Hofeni ndi Pinehasi, cidzakhala cizindikilo kwa iwo, tsiku limodzi adzafa iwo onse awiri.
35 Ndipo ndidzadziukitsira wansembe wokhulupirika, amene adzacita monga cimene ciri mumtima mwanga ndi m'cifuniro canga; ndipo ndidzammangira nyumba yokhazikika, ndipo iyeyu adzayenda pamaso pa wodzozedwa wanga masiku onse.
36 Ndipo kudzali kuti yense wakusiyidwa wa m'banja lako adzabwera kwa iye nadzawerama ndi kupempha ndalama ndi cakudya, nadzati, Mundipatsetu nchito yina ya wansembe, kuti ndikaona kakudya.
1 Ndipo mwanayo Samueli anatumikira Yehova pamaso pa Eli. Ndipo masiku aja mau a Yehova anamveka kamodzi kamodzi; masomphenya sanaoneka-oneka.
2 Ndipo kunali nthawi yomweyo Eli atagona m'malo mwace (maso ace anayamba cizirezire osatha kupenya bwino);
3 ndi nyali ya Mulungu isanazime, Samueli nagona m'Kacisi wa Yehova, m'mene munali likasa la Mulungu.
4 Pamenepo Yehova anaitana Samueli; ndipo iye anayankha kuti, Ndiri pano.
5 Ndipo anathamangira kwa Eli nati, Ndine, popeza mwandiitana ine. Ndipo iye anati, Sindinaitana, kagone. Napita iye, nagona,
6 Ndipo Yehova anabwereza kumuitana, ndi kuti, Samueli. Ndipo Samueli anauka, napita kwa Eli, nati, Ndine, pakuti mwandiitana ndithu. Koma iye anayankha, Sindinaitana, mwana wanga; kagone.
7 Koma Samueli sanadziwe Yehova, ndiponso mau a Yehova sanaululidwe kwa iye.
8 Ndipo Yehova anabwereza kumuitana Samueli nthawi yacitatu. Ndipo iye anauka napita kwa Eli, nati, Ndine, pakuti mwandiitana ndithu. Ndipo Eli anazindikira kuti ndiye Yehova amene analikuitana mwanayo.
9 Cifukwa cace Eli anati kwa Samueli, Pita, ukagone; ndipo akakuitananso, ukabvomere, kuti, Nenani, Yehova, popeza mnyamata wanu akumva. Comweco Samueli anakagona m'malo mwace.
10 Ndipo Yehova anabwera, naimapo, namuitana monga momwemo, Samueli, Samueli. Pompo Samueli anayankha, Nenani, popeza mnyamata wanu akumva.
11 Ndipo Yehova ananena ndi Samueli, Taona, ndidzacita mwa Israyeli coliritsa mwini khutu kwa munthu yense wakucimva.
12 Tsiku lija udidzamcitira Eli zonse ndinaneneratu za pa banja lace, kuciyamba ndi kucitsiriza.
13 Popeza ndinamuuza kuti ndidzaweruza nyumba yace kosatha cifukwa ca zoipa anazidziwa, popeza ana ace anadzitengera temberero, koma iye sanawaletsa.
14 Cifukwa cace ndinalumbira kwa banja la Eli, kuti zoipa za banja la Elilo sizidzafafanizidwa ndi nsembe, kapena ndi zopereka, ku nthawi zonse.
15 Ndipo Samueli anagona kufikira m'mawa, natsegula zitseko za nyumba ya Yehova. Ndipo Samueli anaopa kudziwitsa Eli masomphenyawo.
16 Pamenepo Eli anaitana Samueli, nati, Mwana wanga, Samueli. Nati iye, Ndine.
17 Ndipo anati, Anakuuza cinthu canji? Usandibisire ine. Mulungu akulangendi kuonjezapo, ngati undibisira cimodzi ca zonse zija adanena nawe.
18 Ndipo Samueli anamuuza zonse, sanambisira kanthu. Ndipo iye anati, Ndiye Yehova; acite comkomera pamaso pace.
19 Ndipo Samueli anakula, Yehova nakhala naye, osalola kuti mau ace amodzi apite pacabe.
20 Ndipo Aisrayeli onse, kuyambira ku Dani kufikira ku Beereseba anazindikira kuti Samueli anakhazikika akhale mneneri wa Yehova.
21 Ndipo Yehova anaonekanso m'Silo, pakuti Yehova anadziulula kwa Samueli ku Silo, mwa mau a Yehova.
1 Ndipo mau a Samueli anafikira kwa Aisrayeli onse. Ndipo Aisrayeli anaturuka kukaponyana nkhondo ndi Afilisti, namanga zithando zao ku Ebenezeri; Afilistiwo namanga m'Afeki.
2 Ndipo Afilistiwo anandandalitsa nkhondo yao pa Aisrayeli; ndipo pokomana nkhondo Aisrayeli anakanthidwa ndi Afilisti. Ndipo anapha kuthengoko anthu zikwi zinai a khamu lao.
3 Ndipo pamene anthu anafika ku zithandozo, akuru a Israyeli anati, Yehova anatikanthiranji lero pamaso pa Afilisti? Tikadzitengere likasa la cipangano la Yehova ku Silo, kuti likabwera pakati pa ife, lidzatipulumutsa m'dzanja la adani athu.
4 Cifukwa cace anatumiza ku Silo kuti akatenge kumeneko likasalo la cipangano la Yehova wa makamu, wokhala pakati pa akerubi; ndipo ana awiriwo a Eli, Hofeni ndi Pinehasi anali komweko ndi likasa la cipangano la Yehova.
5 Pakufika likasalo la cipangano la Yehova kuzithando, Aisrayeli onse anapfuula ndi mau okweza, kotero kuti dziko linacita cibvomezi.
6 Ndipo Afilistiwo pakumva kubuma pa kupfuula kwao, anati, Phokoso ili la kupfuula kwakukuru ku zithando za Aisrayeli litani? Ndipo anamva kuti likasa la Yehova lidzafika ku zithandozo.
7 Ndipo Afilisti anaopa, pakuti anati, Mulungu wafika kuzithando. Ndipo iwo anati, Tsoka kwa ife! popeza kale lonse panalibe cinthu cotere.
8 Tsoka kwa ife! adzatilanditsa ndani m'manja a milungu yamphamvu imeneyi? Milungu ija inakantha Aaigupto ndi masautso onse m'cipululu ndi yomweyi.
9 Limbikani, ndipo mucite camuna, Afilisti inu, kuti mungakhale akapolo a Ahebri, monga iwowa anali akapolo anu. Citani camuna nimuponyane nao.
10 Ndipo Afilisti anaponyana nao, nakantha Aisrayeli; iwowa nathawira, munthu yense ku hema wace; ndipo kunali kuwapha kwakukuru; popeza anafako Aisrayeli zikwi makumi atatu a oyenda pansi.
11 Ndipo likasa la Mulungu linalandidwa, ndi ana awiri a Eli, Hofeni ndi Pinehasi, anaphedwa.
12 Ndipo munthu wa pfuko la Benjamini anathamanga kucokera ku khamu la ankhondo, nafika ku Silo tsiku lomwelo, ndi zobvala zace zong'ambika, ndi dothi pamutu pace.
13 Pakufika iye, onani, Eli analikukhala pampando m'mbali mwa njira, alikuyang'anira, popeza mtima wace unanthunthumira cifukwa ca likasa la Mulungu, Pamene munthu uja anafika m'mudzimo, nanena izi, a m'mudzi monse analira.
14 Ndipo Eli, pakumva kubuma kwa kulira kwao, anati, Alikupokoseranji? Ndipo munthuyo anafulumira, nadza nauza Eli.
15 Koma Eli anali ndi zaka makumi asanu ndi anai kudza zisanu ndi zitatu; ndipo maso ace anangokhala tong'o osapenya,
16 Ndipo munthuyo anati kwa Eli, Ine ndine amene ndacokera ku khamu la ankhondo, ndipo ndathawa lero ku khamu la ankhondo. Ndipo iye anati, a Nkhondoyo idatani, mwana wanga?
17 Ndipo wakubwera ndi mauyo anayankha, nati, lsrayeli anathawa pamaso pa Afilisti, ndiponso kunali kuwapha kwakukuru kwa anthu, ndi ana anu awiri omwe Hofeni ndi Pinehasi afa, ndipo likasa la Mulungu lalandiwa.
18 Ndipo kunali, pakunena za likasa la Mulungu, iye anagwa cambuyo pa mpando wace pam bali pa cipata, ndi khosi lace linathyoka, nafa iye; popeza anali wokalamba ndi wamkuru thupi. Ndipo adaweruza anthu a Israyeli zaka makumi anai.
19 Ndipo mpongozi wace, mkazi wa Pinehasi, anali ndi mimba, pafupi pa nthawi yace yakuona mwana; ndipo pakumva iye mau akuti likasa la Mulungu linalandidwa, ndi kuti mpongozi wace, ndi mwamuna wace anafa, iyeyu anawerama, nabala mwana; popeza kucira kwace kwamdzera.
20 Ndipo pamene adati amwalire, anthu akazi akukhala naye ananena, Usaope, popeza waona mwana wamwamuna. Koma iye sanayankha, kapena kusamalira.
21 Ndipo iye anamucha dzina la mwanayo Ikabodi, nati, Ulemerero wacoka kwa Israyeli; cifukwa likasa la Mulungu linalandidwa, ndi cifukwa ca mpongozi wace ndi mwamuna wace.
22 Ndipo iye anati, Ulemerero wacoka kwa Israyeli; cifukwa likasa la Mulungu lalandidwa.
1 Ndipo Afilisti anatenga likasa la Mulungu, nacoka nalo ku Ebenezeri, napita ku Asidodi.
2 Ndipo Afilistiwo anatenga likasa la Mulungu, nafika nalo ku nyumba ya Dagoni, naliika pafupi ndi Dagoni.
3 Ndipo pakuuka a ku Asidodi mamawa, taonani Dagoni adagwa pansi, nagona cafufumimba patsogolo pa likasa la Yehova. Ndipo iwo anatenga Dagoni namuimikanso m'malo mwace.
4 Ndipo m'mawa mwace polawirira, taonani, Dagoni adagwa pansi, nagona cafufumimba patsogolo pa likasa la Yehova; ndipo mutu wace ndi zikhato zonse ziwiri za manja ace zinagona zoduka paciundo; Dagoni anatsala thupi lokha.
5 Cifukwa cace angakhale ansembe, angakhale ena akulowa m'nyumba ya Dagoni, palibe woponda pa ciundo ca Dagoni ku Asidodi, kufikira lero lino.
6 Koma Yehova anabvuta iwo a ku Asidodi ndi dzanja lace, nawaononga, nawazunza ndi mafundo, m'Asidodi ndi m'miraga yace.
7 Ndipo pamene anthu a ku Asidodi anaona kuti ncomweco, anati iwowa, Likasa la Mulungu wa Israyeli lisakhalitse ndi ife; popeza dzanja lace litiwawira ife, ndi Dagoni mulungu wathu.
8 Cifukwa cace anatumiza mithenga, nasonkhanitsa mafumu onse a Afilisti, nati, Ticite nalo ciani likasa la Mulungu wa Israyeli? Ndipo anati, Anyamule likasa la Mulungu kunka nalo ku Gati, Ndipo ananyamula likasalo la Mulungu wa Israyeli, napita nalo kumeneko.
9 Ndipo kunali atafika nalo, dzanja la Yehova linatsutsa mudziwo ndi kusautsa kwakukuru; ndipo anazunza anthu a mudziwo, akuru ndi ang'ono; ndi mafundo anawabuka.
10 Cifukwa cace anatumiza likasa la Mulungu ku Ekroni. Ndipo kunali pofika likasalo ku Ekroni, a ku Ekroni anapfuula nati, Anadzatitulira likasa la Mulungu wa Israyeli, kutipha ife ndi ana athu.
11 Cifukwa cace anatumiza, nasonkhanitsa mafumu onse a Afilisti, ndipo iwowa anati, Cotsani likasa la Mulungu wa Israyeli, lipitenso kumalo kwace, kuti lingationonge ife, ndi anthu athu; pakuti kunali kusautsa koopsa m'mudzi monse; dzanja la Mulungu linabvutadi pamenepo.
12 Ndipo amene anapanda kufa anagwidwa ndi mafundowo; ndi kulira kwa mudziwo kunakwera kumwamba.
1 Ndipo likasa la Yehova linakhala ku dziko la Afilisti miyezi isanu ndi iwiri.
2 Ndipo Afilistiwo anaitana ansembe ndi oombeza, nati, Ticitenji ndi likasa la Yehova? mutidziwitse cimene tilitumize naco kumalo kwace.
3 Ndipo iwo anati, Ngati mulitumiza kwina likasa la Mulungu wa Israyeli, musalitumize lopanda kanthu; koma makamaka mulibweze ndi nsembe yoparamula, mukatero mudzaciritsidwa, ndi kudziwa cifukwa cace dzanja lace liri pa inu losacoka.
4 Ndipo iwo aja anati, Tidzambwezera nsembe yoparamula yanji? Ndipo iwo anati, Mafundo asanu agolidi, ndi mbewa zisanu zagolidi, monga mwa ciwerengo ca mafumu a Afilisti; popeza kusauka kumodzi kunali pa inu nonse, ndi pa mafumu anu.
5 Cifukwa cace muzipanga zifanizo za mafundo anu, ndi zifanizo za mbewa zanu zimene ziipitsa dziko; ndipo mucitire ulemu Mulungu wa lsrayeli; kuti kapena adzaleza dzanja lace pa inu, ndi pa milungu yanu, ndi pa dziko lanu.
6 Mulikuumitsiranji mitima yanu, monga Aaigupto ndi Farao anaumitsa mitima yao? Kodi iwo sana lola anthuwo amuke, iye atacita kodabwitsa pakati pao, ndipo anamuka?
7 Cifukwa cace tsono, tengani, nimukonze gareta latsopano, ndi ng'ombe ziwiri zamkaka, zosalawa goli cikhalire, ndipo mumange ng'ombezo pagareta, muzicotsere ana ao kunka nao kwanu;
8 ndipo mutenge likasa la Yehova, nimuliike pagaretapo; nimuike zokometsera zagolidi, zimene muzipereka kwa iye ngati nsembe yoparamula, m'bokosi pam bali pace; nimulitumize licoke.
9 Ndipo muyang'anire, ngati likwera pa njira ya malire ace ace ku Betisemesi, iye anaticitira coipa ici cacikuru; koma likapanda kutero, tidzadziwapo kuti dzanja limene linatikantha, siliri lace; langotigwera tsokali.
10 Ndipo anthuwo anatero; natenga ng'ombe ziwiri zamkaka, nazimanga pagareta, natsekera anao kwao;
11 naika likasa la Yehova pagaretapo, ndi bokosi m'mene munali mbewa zagolidi ndi zifanizo za mafundo ao.
12 Ndipo ng'ombezo zinatsata njira yolunjika ku Betisemesi, niziyenda mumseu, zirikulira poyenda; sizinapambukira ku dzanja lamanja, kapena kulamanzere; ndipo mafumu a Afilisti anazitsatira kufikira ku malire a Betisemesi.
13 Ndipo a ku Betisemesi analikumweta tirigu wao m'cigwamo; natukula maso ao, naona likasalo, nakondwerapakuliona.
14 Ndipo garetalo linafika m'munda wa Yoswa wa ku Betisemesi, ndi kuima momwemo, pa mwala waukuru; ndipo anawaza matabwa a garetalo, nazipereka ng'ombezo nsembe yopsereza kwa Yehova.
15 Ndipo Alevi anatsitsa likasa la Yehova, ndi bokosi linali nalo, m'mene munali zokometsera zagolidi, naziika pa mwala waukuruwo; ndipo anthu a ku Betisemesi anapereka nsembe zopsereza, naphera nsembe kwa Yehova tsiku lomwelo.
16 Ndipo pamene mafumu asanu a Afilisti anaonerako, anabwerera kunka ku Ekroni tsiku lomwelo.
17 Ndipo amenewa ndiwo mafundo agolidi amene anabwezera kwa Yehova akhale nsembe yoparamula, kwa Asidodi limodzi, kwa Gaza limodzi, kwa Asikeloni limodzi, kwa Gati limodzi, kwa Ekroni limodzi;
18 ndiponso mbewa zagolidi, monga ciwerengo ca midzi yonse ya mafumu asanu a Afilisti, midzi ya malinga, ndi midzi ya kumiraga; kufikira ku mwala waukuru, adaikapo likasa la Yehova; mwalawo ulipobe kufikira lero m'munda wa Yoswa wa ku Betisemesi.
19 Ndipo Mulungu anakantha anthu a ku Betisemesi, cifukwa anasuzumira m'likasa la Yehova, anakantha anthu zikwi makumi asanu; ndipo anthu analira maliro, cifukwa Yehova anawakantha anthuwo ndi makanthidwe akuru.
20 Ndipo a ku Betisemesi anati, Akhoza ndani kuima pamaso pa Yehova, Mulungu Woyera uyu? Ndipo adzakwera kwa yani pakuticokera ife?
21 Ndipo anatumiza mithenga kwa anthu a ku Kiriati-yearimu, nati, Afilisti anabwera nalo likasa la Yehova, mutsike; ndi kukwera nalo kwanu.
1 Ndipo anthu a ku Kiriati-yearimu anabwera, natenga likasa la Yehova, nafika nalo m'nyumba ya Abinadabu paphiri; napatula mwana wace wamwamuna Eleazeri kuti asunge likasa la Yehova.
2 Ndipo kunali, kuti likasalo linakhala nthawi yaikuru m'Kiriati-yearimu; popeza linakhalako zaka makumi awiri; ndipo banja lonse la Israyeli linalirira Yehova.
3 Ndipo Samueli analankhula ndi banja lonse la Israyeli nati, Ngati mukuti mubwerere kunka kwa Yehova ndi mitima yanu yonse, cotsani pakati pa inu milungu yacilendo, ndi Asitaroti, nimukonzere Yehova mitima yanu, ndi kumtumikira iye yekha; mukatero, iye adzakupulumutsani m'manja a Afilisti.
4 Pomwepo ana a Israyeli anacotsa. Abaala ndi Asitaroti, natumikira Yehova yekha.
5 Ndipo Samueli anati, Musonkhanitse Aisrayeli onse ku Mizipa, ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.
6 Ndipo anaunjikana ku Mizipa, natunga madzi, nawatsanula pamaso pa Yehova, nasala cakudya tsiku lija, nati, Tinacimwira Yehova. Ndipo Samueli anaweruza ana a Israyeli m'Mizipa.
7 Ndipo pamene Afilisti anamva kuti Aisrayeli anasonkhana pamodzi ku Mizipa, mafumu a Afilisti anakwera kukayambana ndi Aisrayeli. Ndipo Aisrayeli pakumva ici, anacita mantha ndi Afilistiwo.
8 Ndipo ana a Israyeli anati kwa Samueli, Musaleke kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti iye atipulumutse m'manja a Afilistiwo.
9 Ndipo Samueli anatenga mwana wa nkhosa woyamwa, nampereka wathunthu kwa Yehova, nsembe yopsereza; ndipo Samueli anapempherera Israyeli kwa Yehova; ndipo Yehova anambvomereza.
10 Ndipo pamene Samueli analikupereka nsembe yopserezayo, Afilisti anayandikira kuti aponyane ndi Aisrayeli; koma tsiku lomwe lija Yehova anagunda ndi kugunda kwakukuru pa Afilistiwo, nawapolonganitsa. Ndipo anakanthidwa pamaso pa Aisrayeli.
11 Ndipo Aisrayeli anaturuka ku Mizipa, nathamangira Afilisti, nawakantha mpaka anafika pansi pa Betikara.
12 Pamenepo Samueli anatenga mwala nauimika pakati pa Mizipa ndi Seni, naucha dzina lace. Ebenezeri, nati, Kufikira pano Yehovaanatithandiza.
13 Comweco anagonjetsa Afilisti, ndino iwo sanatumphanso malire a Israyeli ndipo dzanja la Yehova linasautsa Afilisti masiku onse a Samueli.
14 Ndipo midzi ya Israyeli imene Afilisti adailanda kale inabwezedwa kwa Aisrayeli, kuyambira ku Ekroni kufikira ku Gati; ndi Aisrayeli analanditsa miraga yao m'manja a Afilisti. Ndipo pakati pa Aisrayeli ndi Aamori panali mtendere;
15 ndipo Samueli anaweruza Israyeli masiku onse a moyo wace.
16 Ndipo anayenda cozungulira caka ndi caka ku Beteli, ndi ku Giligala, ndi ku Mizipa; naweruza Israyeli m'malo onse amenewa.
17 Ndipo anabwera ku Rama, pakuti nyumba yace inali kumeneko; ndipo pamenepo anaweruza Israyeli; namangapo guwa la nsembe la Yehova.
1 Ndipo kunali, pamene Samueli anakalamba, anaika ana ace amuna akhale oweruza a Israyeli.
2 Dzina la mwana wace woyamba ndiye Yoeli, ndi dzina la waciwiri ndiye Abiya; ndiwo oweruza a ku Beereseba.
3 Ndipo ana ace sanatsanza makhalidwe ace, koma anapambukira ku cisiriro, nalandira cokometsera mlandu, naipitsa kuweruza.
4 Pamenepo akuru onse a Israyeli anasonkhana, nadza kwa Samueli ku Rama;
5 nanena naye, Taonani, mwakalamba, ndipo ana anu satsanza makhalidwe anu; tsono, mutilongere mfumu kuti ikatiweruze, monga umo mucitidwa m'mitundu yonse ya anthu.
6 Koma cimeneci sicinakondweretsa Samueli, pamene iwo anati, Tipatseni mfumu kuti itiweruze. Ndipo Samueli anapemphera kwa Yehova.
7 Ndipo Yehova ananena ndi Samueli, Umvere mau onse anthuwo alikulankhula nawe; popeza sindiwe anakukana, koma ndine anandikana, kuti ndisakhale mfumu yao.
8 Monga nchito zao zonse anazicita kuyambira tsiku lija ndinawaturutsa ku Aigupto, kufikira lero lino kuti anandisiya Ine, natumikira milungu yina, momwemo alikutero ndi iwenso.
9 Cifukwa cace tsono umvere mau ao koma uwacenjeze kolimba, ndi kuwadziwitsa makhalidwe ace a mfumu imene idzawaweruza.
10 Ndipo Samueli anauza anthu akumpempha iye mfumu mau onse a Yehova,
11 Nati, Awa ndi makhalidwe a mfumu imene idzaweruza inu; idzatenga ana anu amuna, akhale akusunga magareta, ndi akavale ace; ndipo adzathamanga ndi kutsogolera magareta ace;
12 idzawaika akhale otsogolera cikwi, ndi otsogolera makumi asanu; ndipo idzaika ena kulima minda yace, ndi kutema dzinthu zace, ndi kumpangira zipangizo za nkhondo, ndi zipangizo za magareta.
13 Ndipo idzatenga ana anu akazi apange zonunkhira, naphikire, naumbe mikate.
14 Ndipo idzalanda minda yanu, ndi minda yamphesa yanu, ndi minda yaazitona, inde minda yoposayo, nidzaipatsa anyamata ace.
15 Ndipo idzatenga limodzi la magawo khumi la mbeu zanu, ndi la minda yanu yamphesa, nidzalipatsa akapitao ace, ndi anyamata ace.
16 Ndipo idzatenga akapolo anu, ndi adzakazi anu, ndi anyamata anu okongola koposa, ndi aburu anu, nidzawagwiritsa nchito yace.
17 Idzatenga limodzi la magawo khumi la zoweta zanu; ndipo inu mudzakhala akapoloace.
18 Ndipotsiku lija mudzapfuula cifukwa ca mfumu yanu munadzisankhira nokha; koma Yehova sadzayankha inu tsiku lijalo.
19 Koma anthu anakana kumvera mau a Samueli; nati, Iai, koma tifuna kukhala nayo mfumu yathu;
20 kuti ifenso tikafanane nao anthu a mitundu yonse; kuti mfumu yathuyo ikatiweruzire, ndi kuturuka kutitsogolera, ndi kuponya nafe nkhondo zathu.
21 Ndipo Samueli anamva mau onse a anthuwo, nawafotokozanso m'makutu a Yehova.
22 Ndipo Yehova anati kwa Samueli, Umvere mau ao, nuwalongere mfumu, Ndipo Samueli anati kwa amuna a Israyeli, Mupite, munthu yense ku mudziwace.
1 Ndipo panali munthu Mbenlamlni, dzina lace ndiye Kisi, mwana wa Abiyeli, mwana wa Zerori, mwana wa Bekorati, mwana wa Afiya, mwana wa Mbenjamini, ndiye ngwazi.
2 Iye anali ndi mwana wamwamuna dzina lace Sauli, mnyamata wokongola; pakati pa anthu onse a Israyeli panalibe wina wokongola ngati iye; anali wamtali, anthu onse ena anamlekeza m'cifuwa.
3 Ndipo aburu a Kisi, atate wa Sauli, analowerera. Ndipo Kisi anati kwa Sauli mwana wace, Utenge mnyamata mmodzi, nunyamuke, kukafuna aburuwo.
4 Ndipo anapyola dziko lamapiri la Efraimu, napyola dziko la Salisa, koma sanawapeza; pamenepo anapyolanso dziko la Salimu; koma panalibe pamenepo, napyola dziko la Abenjamini, osawapeza.
5 Pamene anafika ku dziko la Zufi, Sauli anamuuza mnyamata amene anali naye, kuti, Tiye tibwerere; kuti atate wanga angaleke kusamalira aburuwo, ndi kutenga nkhawa cifukwa ca ife.
6 Koma ananena naye, Onatu, m'mudzi muno muli munthu wa Mulungu, ndiye munthu anthu amcitira ulemu; zonse azinena zicitika ndithu; tiyeni tipite komweko, kapena adzakhoza kutidziwitsa zimene tirikuyendera.
7 Ndipo Sauli ananena ndi mnyamata wace, Koma taona, tikapitako nmtengere ciani munthuyo? popeza mkate udatha m'zotengera zathu, ndiponso tiribe mphatso yakumtengera munthu wa Mulungu, tiri naco ciani?
8 Ndipo mnyamatayo anayankhanso kwa Sauli nati, Onani m'dzanja langa muli limodzi la magawo anai a sekeli wa siliva; ndidzampatsa munthu wa Mulungu limeneli kuti atiuze njira yathu.
9 Kale m'Israyeli, munthu akati afunse kwa Mulungu, adafotero kuti, Tiyeni tipite kwa mlauliyo; popeza iye wochedwa mneneri makono ano, anachedwa mlauli kale.
10 Pamenepo Sauli anati kwa mnyamata wace, Wanena bwino; tiye tipite. Comweco iwowa anapita kumudzi kumene kunali munthu wa Mulunguyo.
11 Pakukwera kumudziko anapeza anthu akazi alikuturuka kuti akatunge madzi, nanena nao, Mlauliyo alipo kodi?
12 Ndipo anawayankha nati, Alipo; onani ali m'tsogolo mwanu; fulumirani pakuti wabwera lero kumudzi kuno; popeza lero anthu akuti aphere nsembe pamsanje;
13 mutafika m'mudzi, pomwepo mudzampeza, asanakwere kumsanje kukadya; pakuti anthu sadzadya, koma iye atafika ndipo; pakuti iye amadalitsa nsembeyo; ndipo atatero oitanidwawo amadya. Cifukwa cace kwerani; popeza nthawi yino mudzampeza.
14 Ndipo iwowa anakwera kumudzi; ndipo m'mene analowa m'mudzimo, onani, Samueli anaturukira pali Iwo, kuti akakwere kumsanje.
15 Ndipo Yehova anaululiratu m'khutu la Samueli dzulo lace la tsiku limene Sauli anabwera, kuti,
16 Mawa, monga dzuwa lino, ndidzakutumizira munthu wocokera ku dziko la Benjamini, udzamdzoza iye akhale mtsogoleri wa anthu anga Israyeli, kuti akawapulumutse anthu anga m'manja a Afilisti; pakuti Ine ndinapenya pa anthu anga, popeza kulira kwao kunandifika Ine.
17 Ndipo pamene Samueli anaona Sauli, Yehova anati kwa iye, Ona munthu amene ndinakuuza za iye! ameneyu adzaweruza anthu anga.
18 Pomwepo Sauli anayandikira kwa Samueli pakati pa cipata, nati, Mundidziwitse nyumba ya mlauliyo iri kuti.
19 Ndipo Samueli anayankha Sauli nati, Inendinemlauliyo. Kwera, batsogola kumsanje, pakuti mudzadya ndi ine lero; ndipo m'mawa ndidzakulola upite, ndi kukudziwitsa zonse ziri mumtima mwako.
20 Za aburu ako atatayika adapita masiku atatu, usalingalirenso iwowa; pakuti anapezedwa. Ndipo cifuniro conse ca Israyeli ciri kwa yani? Si kwa iwe ndi banja lonse la atate wako?
21 Ndipo Sauli anayankha nati, Sindiri Mbenjamini kodi, wa pfuko laling'ono mwa Israyeli? Ndiponso banja lathu nlocepa pakati pa mabanja onse a pfuko la Benjamini? Potero mulankhula bwanji mau otere ndi ine?
22 Ndipo Samueli anatenga Sauli ndi mnyamata wace, napita nao ku cipinda ca alendo, nawakhalitsa pa malo a ulemu pakati pa oitanidwa onse; ndiwo anthu monga makumi atatu.
23 Ndipo Samueli ananena ndi wophika, Tenga nyama ndinakupatsa, ndi kuti, Ibakhala ndi iwe.
24 Ndipo wophikayo ananyamula mwendo ndi mnofu wace, nauika pamaso pa Sauli. Ndipo Samueli anati, Onani cimene tinakuikirani muciike pamaso panu, nudye; pakuti ici anakuikirani kufikira nthawi yonenedwa, popeza ndinati, Ndinaitana anthuwoo Comweco Sauli anadya ndi Samueli tsiku lija.
25 Ndipo pamene anatsika kumsanje kulowanso kumudzi, iye anakamba ndi Sauli pamwamba pa nyumba yace.
26 Ndipo anauka mamawa; ndipo kutaca, Samueli anaitana Sauli ali pamwamba pa nyumba, nati, Ukani kuti ndikuloleni mumuke. Ndipo Sauli anauka, naturuka onse awiri, iye ndi Samueli, kunka kunja.
27 Ndipo pamene analikutsika polekeza mudzi, Samueli ananena ndi Sauli, Uzani mnyamatayo abatsogola; napita iyeyo. Koma inu muime pano, kuti ndikumvetseni mau a Mulungu.
1 Pamenepo Samueli anatenga nsupa ya mafuta, nawatsanulira pamutu pace, nampsompsona iye, nati, Sanakudzozani ndi Mulungu kodi, mukhale mfumu ya pa colowa cace?
2 M'mene talekana lero, mudzakomana ndi anthu awiri pa manda a Rakele, pa malire a Benjamini ku Zeliza; iwo ndiwo adzanena nanu, Aburu aja munakafuna, anapezedwa; ndipo onani, atate wanu analeka kulingalira aburuwo, koma alikulingalira za inu, ndi kuti, Ndidzacita ciani, cifukwa ca mwana wanga?
3 Mukapitirira pamenepo tsono ndi kufika ku mtengo wathundu wa ku Tabori, kumeneko adzakomana nanu anthu atatu akukwera kwa Mulungu ku Beteli, wina wonyamula ana a mbuzi atatu, wina mikate itatu, wina thumba la vinyo.
4 Iwowa adzakulankhulani, ndi kukupatsani mikate iwiri; imeneyi mudzailandira m'manja mwao.
5 Ndipo m'tsogolo mwace mudzafika ku phiri la Mulungu, kumene kuli kaboma ka Afilisti; ndipo kudzali kuti pakufika inu kumudziko mudzakomana ndi gulu la aneneri, alikutsika kumsanje ndi cisakasa, ndi lingaka, ndi toliro, ndi zeze, pamaso pao; iwo adzanenera;
6 ndipo Mzimu wa Yehova udzagwera inu kolimba, nanunso mudzanenera pamodzi nao, nimudzasandulika munthu wina.
7 Ndipo zitakufikirani zizindikilo izi mudzacita monga mudzaona pocita, pakuti Mulungu ali nanu.
8 Ndipo mudzatsika patsogolo pa ine kunka ku Giligala; ndipo, taonani, ndidzatsikira kwa inu kukapereka zopsereza, ndi kuphera nsembe zamtendere. Mutsotsepo masiku asanu ndi awiri kufikira ndikatsikira kwa inu ndi kukudziwitsani cimene mudzacita.
9 Ndipo kunali, pamene iye anapotoloka kuti alekane ndi Samueli, Mulungu anampatsa mtima wina watsopano; ndipo zizindikilo zija zonse zinacitika tsiku lija.
10 Ndipo pamene anafika kucitunda kuja, onani, gulu la aneneri linakomana naye; ndi Mzimu wa Mulungu unamgwera mwamphamvu, iye nanenera pakati pao,
11 Ndipo kunali, kuti onse amene anamdziwiratu kale, pakuona ici cakuti, onani, iye ananenera pamodzi ndi aneneri, anati wina ndi mnzace, Ici nciani cinamgwera mwana wa Kisi? Kodi Saulinso ali mwa aneneri?
12 Ndipo munthu wina wa komweko anayankha nati, Ndipo atate wao ndiye yani? Cifukwa cace mauwa anakhala ngati mwambi, Kodi Saulinso ali mwa aneneri?
13 Ndipo pamene adatha kunenera anafika kumsanjeko.
14 Ndipo mbale wa atate wace wa Sauli ananena kwa iye ndi mnyamata wace, Munanka kuti? Ndipo iye anati, Kukafuna aburuwo; ndipo pakuona kuti sitinawapeza, tinadza kwa Samueli.
15 Ndipo mbale wa atate wa Sauli anati, Undiuze cimene Samueli analankhula nawe.
16 Ndipo Sauli anati kwa mbale wa atate wace, Anatiuza momveka kuti aburuwo anapezedwa kale. Koma sanamdziwitsa mau aja Samueli ananena zaufumuwo.
17 Ndipo Samueli anaitana anthu onse asonkhane kwa Yehova ku Mizipa;
18 nanena ndi ana a Israyeli, Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli kuti, Ine ndinaturutsa Israyeli m'Aigupto, ndipo ndinakupulumutsani m'manja a Aaigupto, ndi m'manja a maufumu onse anakusautsani;
19 koma lero inu mwakana Mulungu wanu amene anakupulumutsani yekha m'matsoka anu onse, ndi m'masautso anu; ndipo munanena naye, Koma mutipatse mfumu. Cifukwa cace tsono mudzionetse pamaso pa Mulungu mafuko mafuko, ndi magulu magulu.
20 Comweco Samueli anayandikizitsa mafuko onse a Israyeli, ndipo pfuko la Benjamini linasankhidwa.
21 Nayandikizitsa pfuko la Benjamini, banja ndi banja, ndipo banja la Amatiri linasankhidwa; nasankhidwa Sauli mwana wa Kisi. Koma pamene anamfuna, anapeza palibe.
22 Cifukwa cace anaonjeza kufunsa Yehova, Watsala wina kodi woyenera kubwera kuno? Ndipo Yehova anati, Onani, alikubisala pakati pa akatundu.
23 Ndipo anathamanga, namtenga komweko; ndipo iye pamene anaima pakati pa anthuwo, anali wamtali koposa anthu onse anamlekeza m'cifuwa.
24 Ndipo Samueli ananena ndi anthu onse, Mumuona kodi iye amene Yehova anamsankha, kuti palibe wina wakufanana naye pakati pa anthu onse? Ndipo anthu onse anapfuula, kuti, Akhale ndi moyo mfumuyo.
25 Pamenepo Samueli anafotokozera anthu macitidwe a ufumu, nawalembera m'buku, nalisunga pamaso pa Yehova. Ndipo Samueli anauza anthu onse amuke, yense ku nyumba yace,
26 Ndi Sauli yemwe anamuka ku nyumba yace ku Gibeya; ndipo am'khamu anatsagana naye iwo amene Mulungu adakhudza mitima yao.
27 Koma oipa ena anati, Uyu adzatipulumutsa bwanji? Ndipo anampeputsa, osakampatsa mtulo. Koma iye anakhala cete.
1 Pamenepo Nahasi M-amoni anakwera, namanga Yabezi Gileadi zithando; ndipo anthu onse a ku Yabezi anati kwa Nahasi, Mupangane cipangano ndi ife, ndipo tidzakutumikirani inu.
2 Ndipo Nahasi Mamoni ananena nao, Ndidzapangana nanu, ngati mulola kuti maso a ku dzanja lamanja anu onse akolowoledwe; potero ndidzanyazitsa Aisrayeli onse.
3 Ndipo akuru a ku Yabezi ananena naye, Mutipatse masiku asanu ndi awiri, kuti titumize mithenga m'malire onse a Israyeli; ndipo pakapanda kuoneka wotipulumutsa ife, tidzaturukira kwa inu.
4 Tsono mithengayo inafika ku Gibeya kwa Sauli, nalankhula mau amenewa m'makutu a anthu; ndipo anthu onse anakweza mau, nalira misozi.
5 Ndipo, onani, Sauli anacokera kumunda alikutsata ng'ombe; nati Sauli, Coliritsa anthu misozi nciani? Ndipo anamuuza mau a anthu a ku Yabezi.
6 Ndipo mzimu wa Mulungu unamgwera Sauli mwamphamvu, pamene anamva mau awa, ndi mkwiyo wace unayaka kwambiri.
7 Natenga ng'ombe ziwiri nazidula nthuli nthuli, nazitumiza m'malire monse mwa Israyeli, ndi dzanja la mithenga, nati, Amene sakudza pambuyo pa Sauli ndi pa Samueli, adzatero nazo ng'ombe zace. Ndipo kuopsa kwa Yehova kunawagwera anthu, naturuka ngati munthu mmodzi.
8 Ndipo anawawerenga ku Bezeki; ndipo ana a Israyeli anali zikwi mazana atatu, ndi anthu a Yuda ndiwo zikwi makumi atatu.
9 Ndipo anati kwa mithenga inadzayi, Muzitero kwa anthu a ku Yabezi Gileadi, Mawa litatentha dzuwa, mudzaona cipulumutso. Ndipo mithenga inadza niuza a ku Yabezi; nakondwara iwowa.
10 Cifukwa cace anthu a ku Yabezi anati, Mawa tidzaturukira kwa inu, ndipo mudzaticitira cokomera inu.
11 Ndipo m'mawa mwace Sauli anagawa anthu magulu atatu; ndipo iwowa anafika pakati pa zithandozo m'ulonda wa mamawa, nakantha Aamoni kufikira kutentha kwa dzuwa. Ndipo otsalawo anabalalika, osatsala pamodzi ngakhale awiri.
12 Ndipo anthu anati kwa Samueli, Ndani iye amene anati, Kodi Sauli adzatiweruza ife? tengani anthuwo kuti tiwaphe.
13 Koma Sauli anati, Sadzaphedwa lero munthu; pakuti lero Yehova anacita cipulumutso m'lsrayeli.
14 Ndipo Samueli ananena kwa anthuwo, Tiyeni tipite ku Giligala, kukonzanso ufumu kumeneko.
15 Ndipo anthu onse anapita ku Giligala; ndi kumeneko analonga Sauli mfumu pamaso pa Yehova m'Giligala; ndi pamenepo anaphera nsembe zoyamika pamaso pa Yehova; ndi pomwepo Sauli ndi anthu onse a Israyeli anakondwera kwakukuru.
1 Ndipo Samueli anauza Aisrayeli onse, kuti, Onani dani ndinamvera mau anu mwa zonse munalankhula ndi ine, ndipo ndinakulongerani mfumu.
2 Ndipo tsopano, siyi mfumu idzayendabe pamaso panu; ndipo ine ndine wokalamba waimvi; ndipo, onani, ana anga amuna ali nanu, ndipo ine ndinayendabe pamaso panu kuyambira ubwana wanga kufikira lero.
3 Ndikalipo ine; citani umboni wonditsutsa pamaso pa Yehova, ndi pamaso pa wodzozedwa wace; ndinalanda ng'ombe ya yani? kapena ndinalanda buru wa yani? ndinanyenga yani? ndinasautsa yani? ndinalandira m'manja mwa yani cokometsera mlandu kutseka naco maso anga? ngati ndinatero ndidzacibwezera kwa inu.
4 Ndipo iwo anati, Simunatinyenga, kapena kutisautsa, kapena kulandira kanthu m'manja mwa wina ali yense.
5 Ndipo iye ananena nao, Yehova ali mboni yanu, ndi wodzozedwa wace ali mboni lero kuti simunapeza kanthu m'dzanja langa, Nati iwo, iye ali mboni.
6 Ndipo Samueli ananena ndi anthuwo, Yehova ndiye amene anaika Mose ndi Aroni, naturutsanso makolo anu m'dziko la Aigupto,
7 Cifukwa cace tsono, imani pano, kuti ndiweruzane nanu pamaso pa Yehova za nchito zonse zolungama za Yehova, anakucitirani inu ndi makolo anu.
8 Pamene Yakobo anafika ku Aigupto, ndi makolo anu anapemphera kwa Yehova, Yehova anatumiza Mose ndi Aroni, amene anaturutsa makolo anu m'Aigupto, nawakhalitsa pamalo pano,
9 Koma iwowa anaiwala Yehova Mulungu wao, iye nawapereka m'dzanja la Sisera kazembe wa gulu la Hazori, ndi m'dzanja la Afilisti, ndi m'dzanja la mfumu ya Moabu, iwo naponyana nao.
10 Ndipo anapemphera kwa Yehova, kuti, Tinacimwa, popeza tinasiya Yehova, ndi kutumikira Abaala ndi Asitaroti, koma mutipulumutse tsopano m'manja a adani anthu, ndipo tidzakutumikirani Inu.
11 Ndipo Yehova anatumiza Yerubaala, ndi Bedani, ndi Yefita, ndi Samueli, napulumutsa inu m'manja mwa adani anu pozungulira ponse, ndipo munakhala mosatekeseka.
12 Ndipo pamene munaona kuti Nahasi mfumu ya ana a Amoni inadza kuponyana nanu, munanena ndi ine, Koma mfumu itiweruze; ngakhale mfumu yanu ndiye Yehova Mulungu wanu.
13 Cifukwa cace siyi mfumu imene munaisankha, imene munandipempha; ndipo taonani, Yehova anakuikirani mfumu.
14 Mukaopa Yehova ndi kumtumikira ndi kumvera mau ace, ndi kusakana lamulo lace la Yehova, ndipo inu ndi mfumu imene iweruza inu mukadzatsata Yehova Mulungu wanu, cabwino.
15 Koma mukapanda kumvera mau a Yehova, ndi kupikisana ndi lamulo la Yehova, dzanja la Yehova lidzatsutsana nanu, monga linatsutsana ndi makolo anu.
16 Cifukwa cace tsono, imani pano, muone cinthu ici cacikuru Yehova adzacicita pamaso panu.
17 Si nyengo yakumweta tirigu lero kodi? Ndidzaitana kwa Yehova, kuti atomize bingu ndi mvula; ndipo mudzazindikira ndi kuona kuti coipa canu munacicita pamaso pa Yehova ndi kudzipemphera mfumu, ncacikuru.
18 Momwemo Samueli anaitana kwa Yehova; ndipo Yehova anatumiza bingu ndi mvula tsiku lomwelo; ndipo anthu onse anaopa kwambiri Yehova ndi Samueli.
19 Ndipo anthu onse ananena ndi Samueli, Mupempherere akapolo anu kwa Yehova Mulungu wanu, kuti tingafe; popeza pamwamba pa zoipa zathu zonse tinaonjeza coipa ici, cakuti tinadzipemphera mfumu.
20 Ndipo Samueli ananena kwa anthuwo, Musaope; munacitadi coipa ici conse, koma musaleka kutsata Yehova, koma mutumikire Yehova ndi mtima wanu wonse;
21 musapambukire inu kutsata zinthu zacabe, zosapindulitsa, zosapulumutsa, popeza ziri zopanda pace.
22 Pakuti Yehova sadzasiya anthu ace cifukwa ca dzina lace lalikuru; pakuti kudamkomera Yehova kukuyesani inu anthu a iye yekha.
23 Ndipo inenso, kukhale kutali ndi ine, kucimwira Yehova ndi kuleka kukupemphererani; koma ndidzakulangizani njira yabwino ndi yolungama.
24 Koma mumuope Yehova, ndi kumtumikira koona, ndi mtima wanu wonse; lingalirani zinthu zazikuruzo iye anakucitirani.
25 Koma mukaumirirabe kucita coipa, mudzaonongeka, inu ndi mfumu yanu yomwe.
1 Sauli anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ufumu wace; nakhala mfumu ya Israyeli zaka ziwiri.
2 Pamenepo Sauli anadzisankhira anthu zikwi zitatu a Israyeli; zikwi ziwiri za iwowa zinali ndi Sauli ku Mikimasi, ndi ku phiri la ku Beteli; ndi cikwi cimodzi anali ndi Jonatani ku Gibeya wa ku Benjamini; ndipo anawauza anthu ena onse amuke ku mahema ao.
3 Ndipo Jonatani anathyola kaboma ka Afilisti lokhala ku Geba, ndipo Afilisti anamva za ici. Ndipo Sauli analiza lipenga m'dziko monse, nati, Amve Ahebri.
4 Ndipo Aisrayeli onse anamva kunena kuti Sauli anathyola kaboma ka Afilisti, ndi kuti Afilisti anyansidwa ndi Aisrayeli. Ndipo anthuwo anasonkhana kwa Sauli ku Giligala.
5 Ndipo Afilisti anasonkhana kuti akamenyane ndi Aisrayeli, anali nao magareta zikwi makumi atatu, ndi apakavalo zikwi zisanu ndi cimodzi, ndi anthu akucuruka monga mcenga wa pa dooko la nyanja. Iwowa anakwera namanga zithando ku Mikimasi kum'mawa kwa Betaveni.
6 Pamene anthu a Israyeli anazindikira kuti ali m'kupsinjika, pakuti anthuwo anasauka mtima, anthuwo anabisala m'mapanga, ndi m'nkhalango, ndi m'matanthwe, ndi m'malinga, ndi m'maenje.
7 Ndipo Ahebri ena anaoloka Yordano nafika ku dziko la Gadi ndi Gileadi; koma Sauli akali ku Giligala, ndipo anthu onse anamtsata ndi kunthunthumira.
8 Ndipo iye anatsotsa masiku asanu ndi awiri, monga nthawi anampanga Samueli; koma Samueli sanafika ku Giligala, ndipo anthu anabalalika namsiya Sauli.
9 Pamenepo Sauli anati, Andipatsire kuno nsembe yopsereza, ndi nsembe zoyamika. Ndipo iye anapereka nsembe yopserezayo.
10 Ndipo kunali kuti pakutsiriza iye kupereka nsembe yopserezayo, pomwepo, onani, Samueli anafika. Ndipo Sauli anamcingamira kukamlankhula iye.
11 Ndipo Samueli anati, Mwacitanji? Nati Sauli, Cifukwa ndinaona kuti anthuwo alinkubalalika kundisiya ine, ndi kuti inu simunafika masiku aja tinapangana, ndi kuti Afilisti anasonkhana ku Mikimasi;
12 cifukwa cace ndinati, Afilisti adzatitsikira pane pa Giligala, ndisanapembedze Yehova; potero ndinadzifulumiza, ndi kupereka nsembe yopsereza.
13 Ndipo Samueli ananena ndi Sauli, Munacita kopusa; simunasunga lamulo la Yehova Mulungu wanu, limene iye anakulamulirani; mwenzi Yehova atakhazikitsa nthawi yino ufumu wanu, ukhale pa Israyeli nthawi yosatha.
14 Koma tsopano ufumu wanu sudzakhala cikhalire; Yehova wadzifunira munthu wa pamtima pace; ndipo Yehova wamuika iye akhale mtsogoleri wa anthu ace, cifukwa inu simunasunga cimene Yehova anakulamulirani.
15 Ndipo Samueli anauka nacoka ku Giligala kunka ku Gibeya wa ku Benjamini. Ndipo Sauli anawerenga anthu amene anali naye, monga mazana asanu ndi limodzi.
16 Ndipo Sauli, ndi Jonatani mwana wace, ndi anthu akukhala nao anakhala ku Geba wa ku Benjamini; koma Afilistiwo anali nazo zithando zao ku Mikimasi.
17 Ndipo owawanya anaturuka ku zithando za Afilisti magulu atatu; gulu limodzi linalowa njira yonka ku Ofra, ku dera la Sauli;
18 gulu lina linalowa njira yonka ku Betihoroni; ndi gulu linanso linalowa ku njira ya kumalire, akuyang'ana ku cigwa ca Zeboimu kucipululuko.
19 Ndipo m'dziko lonse la Israyeli simunapezeka wosula; popeza Afilisti adati, Kuti Aisrayeli angadzisulire malupanga kapena mikondo;
20 koma Aisrayeli onse adafotsikira kwa Afilisti, kuti awasaniire munthu yense cikhasu cace, colimira cace, nkhwangwa yace, ndi khasu lace;
21 koma analf nao matupa kukonza makasu, ndi zikhasu ndi makasu a mana ndi nkhwangwazo; ndi kusongola zothwikira.
22 Comweco kunali kuti tsiku lankhondolo sunapezeka mkondo kapena lupanga m'manja a anthu onse anali ndi Sauli ndi Jonatani; koma Sauli yekha ndi Jonatani mwana wace anali nazo.
23 Ndipo a ku kaboma ka Afilisti anaturuka kunka ku mpata wa ku Mikimasi.
1 Ndipo kunali tsiku lina kuti Jonatani mwana wa Sauli ananena ndi mnyamata wonyamula zida zace, Tiye tipite kunka ku kaboma ka Afilisti, tsidya lija. Koma sanauza atate wace.
2 Ndipo Sauli analikukhala m'matsekerezo a Gibeya patsinde pa mtengo wankhangaza uli ku Migroni; ndipo panali naye anthu monga mazana asanu ndi limodzi;
3 ndi Ahiya mwana wa Ahitubi mbale wace wa Ikabodi, mwana wa Pinehasi, mwana wa Eli, wansembe wa Yehova wa ku Silo, wobvala efodi. Ndipo anthuwo sanadziwa kuti Jonatani wacoka.
4 Ndipo pakati pa mipata imene Jonatani anafuna kupitapo kunka ku kaboma ka Afilisti, panali phiri lathanthwe pa mbali yina, ndi phiri lathanthwe pa mbali inzace; ndipo dzina la linalo ndilo Bozezi, ndi la linzace ndilo Sene.
5 Phiri lija linaimirira kuyang'ana kumpoto pandunji pa Mikimasi, ndi linzace kumwera pandunji pa Geba.
6 Ndipo Jonatani ananena ndi mnyamata wonyamula zida zace, Tiye tipite ku kaboma ka osadulidwa awa; kapena Yehova adzatigwirira nchito; pakuti palibe comletsa Yehova kupulumutsa angakhale ndi ambiri kapena ndi owerengeka.
7 Ndipo wonyamula zida zace ananena naye, Citani zonse ziri mumtima mwanu; palukani, onani ndiri pamodzi ndi inu monga mwa mtima wanu.
8 Ndipo Jonatani anati, Taona, ife tidzapita kunka kwa anthuwo, ndipo tidzadziu lula kwa iwo.
9 Akatero ndi ife kuti, Baimani kufikira titsikira kwa inu; tsono tidzaima m'malo mwathu, osakwera kwa iwo.
10 Koma akatero kuti, Kwerani kuno kwa ife, tsono tidzakwera; pakuti Yehova wawapereka m'manja mwathu; ndipo ici cidzatikhalira cizindikilo.
11 Ndipo onse awiri anadziulula kwa a ku kaboma ka Afilistiwo; ndipo Afilistiwo anati, Onani, Ahebri alikuturuka m'mauna m'mene anabisala.
12 Ndipo a ku kabomawo anayankha Jonatani ndi wonyamula zida zace, nati, Kwerani kuno kwa ife, tikuonetseni kanthu. Ndipo Jonatani anauza wonyamula zida zace, Kwera unditsate m'mbuyo, pakuti Yehova wawapereka m'dzanja la Israyeli.
13 Ndipo Jonatani anakwera cokwawa, ndi wonyamula zida zace anamtsata; ndi Afilisti anagwa pamaso pa Jonatani, ndi wonyamula zida zace anawapha pambuyo pace.
14 Kuwapha koyambako, Jonatani ndi wonyamula zida zace, anapha monga anthu makumi awiri, monga ndime ya munda yolima ng'ombe ziwiri tsiku limodzi.
15 Ndipo kunali kunthunthumira kuzithando, kuthengoko, ndi pakati pa anthu onse; a ku kaboma ndi owawanya omwe ananthunthumira; ndi dziko linagwedezeka; comweco kunali kunthunthumira kwakukuru koposa,
16 Ndipo ozonda a Sauli ku Gibeya wa ku Benjamini anayang'ana; ndipo, onani, khamu la anthu linamwazikana, kulowa kwina ndi kwina.
17 Pamenepo Sauli ananena ndi anthu amene anali naye, Awerenge tsopano, kuti tizindikire anaticokera ndani. Ndipo pamene anawerenga, onani Jonatani ndi wonyamula zida zace panalibe.
18 Ndipo Sauli ananena ndi Ahiya, Bwera nalo likasa la Mulungu kuno. Pakuti likasa la Mulungu linali kumeneko masiku aja ndi ana a Israyeli.
19 Ndipo kunali m'mene Sauli anali cilankhulire ndi wansembeyo, phokoso la m'cigono ca Afilisti linacitikabe, nilikula; ndipo Sauli ananena ndi wansembeyo, Bweza dzanja lako.
20 Ndipo Sauli ndi anthu onse amene anali naye anaunjikana pamodzi, naturukira kunkhondoko; ndipo taonani, munthu yense anakantha mnzace ndi lupanga, ndipo panali kusokonezeka kwakukuru.
21 Ndiponso Ahebri akukhala nao Afilisti kale, amene anaturuka m'dziko lozungulira kukaiowa nao kuzithando; iwonso anatembenukira kuti akakhale ndi Aisrayeli amene anali ndi Sauli ndi Jonatani.
22 Anateronso Aisrayeli onse akubisala m'phiri la Efraimu, pakumva kuti Afilisti anathawa, iwo anawapitikitsa kolimba kunkhondoko.
23 Comweco Yehova anapulumutsa Israyeli tsiku lija; ndipo nkhondo inapitirira pa Betaveni.
24 Ndipo Aisrayeli anasauka tsiku lija; pakuti Sauli anawalumbirira, kuti, Atembereredwe iye wakudya kanthu kufikira madzulo, ndikabwezere cilango adani anga. Motero anthu onse anakhala opanda kudya.
25 Ndipo anthu onsewo analowa munkhalango, panali uci pansi.
26 Ndipo pakufika anthuwo m'nkhalangomo, onani, madzi a uci anacuruka; koma panalibe munthu mmodzi anaika dzanja lace pakamwa, pakuti anthuwo anaopa tembererolo.
27 Koma Jonatani sanamva m'mene atate wace analumbirira anthu; cifukwa cace iye ana tam balitsa ndodo ya m'dzanja lace, naitosa m'cisa ca uci, naika dzanja lace pakamwa pace; ndipo m'maso mwace munayera.
28 Ndipo wina wa anthuwo anayankha, nati, Atate wanu analangiza anthu kolimba ndi lumbiro, ndi kuti, Wotembereredwa iye wakudya lero cakudya. Ndipo anthuwo analema.
29 Ndipo Jonatani anati, Atate wanga wabvuta dziko; onani m'maso mwanga mwayera, cifukwa ndinalawako pang'ono uciwu.
30 Koposa kotani nanga, ngati anthu akadadya nakhuta zowawanya anazipeza za adani ao? popeza tsopano palibe kuwapha kwakukuru kwa Afilisti.
31 Ndipo anakantha Afilisti tsiku lija kuyambira ku Mikimasi kufikira ku Ajaloni, ndipo anthu anafoka kwambiri.
32 Ndipo anthuwo anathamangira zowawanyazo, natenga nkhosa, ndi ng'ombe, ndi ana a ng'ombe, naziphera pansi; anthu nazidya ziri ndi mwazi wao.
33 Pamenepo anauza Sauli, kuti, Onani anthu alikucimwira Yehova, umo akudya zamwazi. Ndipo iye anati, Munacita konyenga; kunkhunizani mwala waukuru kwa ine lero.
34 Ndipo Sauli anati, Balalikani pakati pa anthu, nimuwauze kuti abwere kwa ine kuno munthu yense ndi ng'ombe yace, ndi munthu yense ndi nkhosa yace, aziphe pano, ndi kuzidya, osacimwira Yehova ndi kudya zamwazi. Nabwera anthu onse, yense ndi ng'ombe yace, usiku uja naziphera pomwepo.
35 Ndipo Sauli anamangira Yehova guwa la nsembe; limenelo ndilo guwa loyamba iye anamangira Yehova.
36 Ndipo Sauli anati, Tiyeni titsikire usiku kwa Afilistiwo, ndi kuwawawanya kufikira kutayera, tisasiye munthu mmodzi wa iwowa. Ndipo iwo anati, Citani ciri conse cikukomerani. Pamenepo wansembeyo anati, Tisendere kwa Yehova kuno.
37 Ndipo Sauli anafunsira uphungu kwa Mulungu, Nditsikire kodi kwa Afilisti? Mudzawapereka m'dzanja la Israyeli kodi? Koma iye sanamyankha tsiku lomweli.
38 Ndipo Sauli anati, Musendere kuno, inu nonse akuru a anthu; kuti muzindikire ndi kuona m'mene muli coipa ici lero.
39 Pakuti, pali Yehova wakupulumutsa Israyeli, cingakhale ciri m'mwana wanga Jonatani, koma adzafa ndithu. Koma pakati pa anthu onse panalibe mmodzi wakumyankha iye.
40 Ndipo iye ananena ndi Aisrayeli onse, Inu mukhale mbali yina, ndipo me ndi Jonatani mwana wanga tidzakhala mbali yinanso. Ndipo anthuwo ananena ndi Sauli, Citani cimene cikukomerani.
41 Cifukwa cace Sauli ananena ndi Yehova, Mulungu wa Israyeli, muonetse coonadi. Ndipo maere anagwera Sauli ndi Jonatani; koma anthuwo anapulumuka.
42 Ndipo Sauli anati, Mucite maere pakati pa ine ndi Jonatani mwana wanga. Ndipo anagwera Jonatani.
43 Pamenepo Sauli ananena ndi Jonatani, Undiuze cimene unacita. Ndipo Jonatani anamuuza, nati, Zoonadi ndinangolawako uci pang'ono ndi nsonga ya ndodo inali m'dzanja langa: ndipo onani ndiyenera kufa.
44 Pamenepo Sauli anati, Mulungu andilange, naoniezereko, pakuti udzafa ndithu, Jonatani.
45 Ndipo anthuwo ananena ndi Sauli, Kodi Jonatani adzafa, amene anacititsa cipulumutso cacikuru ici m'Israyeli? Musatero. Pali Yehova, palibe tsitsi limodzi la pa mutu wace lidzagwa pansi, pakuti iye anagwirizana ndi Mulungu lero. Comweco anthuwo anapulumutsa Jonatani kuti angafe. Ndipo Sauli analeka kuwapitikitsa Afilistiwo;
46 ndi Afilistiwo anamuka ku malo a iwo okha.
47 Ndipo pamene Sauli atakhazikitsa ufumu wa pa Israyeli, iye anaponyana ndi adani ace onse pozungulira ponse, ndi Moabu, ndi ana a Amoni, ndi Edomu ndi mafumu a Zoba, ndi Afilisti; ndipo pali ponse anapotolokerapo, anawalanga.
48 Ndipo iye anakula mphamvu, nakantha Aamaleki, napulumutsa Aisrayeli m'manja a akuwawawanya.
49 Ndipo ana a Sauli ndiwo Jonatani, ndi Isivi, ndi Malikisuwa; ndi maina a ana akazi ace awm ndi awa: dzina la woyamba ndiye Merabu, ndi dzina la mng'ono wace ndiye Mikala;
50 ndi dzina la mkazi wa Sauli ndi Ahinamu mwana wa Ahimazi; ndi dzina la kazembe wa khamu lankhondo lace ndiye Abineri mwana wa Neri, mbale wace wa atate wa Sauli.
51 Ndipo atate wa Sauli ndiye Kisi; ndipo Neri atate wa Abineri ndiye mwana wa Abiyeli.
52 Ndipo panali nkhondo yowawa ndi Afilisti masiku onse a Sauli; ndipo Sauli pakuona munthu wamphamvu, kapena ngwazi, anamtenga akhale naye.
1 Ndipo Samueli ananena ndi Sauli, Yehova ananditumiza ine kukudzozani mukhale mfumu ya anthu ace Aisrayeli; cifukwa cace tsono mumvere kunena kwa mau a Yehova.
2 Atero Yehova wa makamu, Ndinaonerera cimene Amaleki anacitira Israyeli, umo anamlalira panjira, m'mene iye anakwera kuturuka m'Aigupto.
3 Muka tsopano, nukanthe Amaleki, nuononge konse konse zonse ali nazo, usawalekerere, koma uwaphe mwamuna ndi mkazi, mwana ndi woyamwa, ng'ombe ndi nkhosa, ngamila ndi buru.
4 Ndipo Sauli anamemeza anthu, nawawerenga ku Telayimu, akuyenda pansi zikwi mazana awiri, ndi a kwa Yuda anthu zikwi khumi.
5 Ndipo Sauli anafika ku mudzi wa Amaleki, nalalira kucigwa.
6 Ndipo Sauli anauza Akeni kuti, Mukani, cokani mutsike kuturuka pakati pa Aamaleki, kuti ndingakuonongeni pamodzi ndi iwo; pakuti inu munacitira ana a Israyeli onse zabwino, pakufuma iwo ku Aigupto. Comwece Akeni anacoka pakati pa Aamaleki.
7 Ndipo Sauli anakantha Aamaleki, kuyambira pa Havila, dera la ku Suri; ciri pandunji pa Aigupto.
8 Namtenga wamoyo Agagi, mfumu ya Aamaleki, naononga konse konse anthu onse ndi lupanga lakuthwa.
9 Koma Sauli ndi anthu anamsunga wamoyo Agagi, ndi nkhosa zokometsetsa, ndi ng'ombe, ndi zonenepa zina, ndi ana a nkhosa, ndi zabwino zonse, sadafuna kuzitha psiti; koma zonse zoipa ndi zonyansa anaziononga konse konse.
10 Pamenepo mau a Yehova anafika kwa Samueli, nati,
11 Kundicititsa cisoni kuti ndinaika Sauli akhale mfumu; pakuti wabwerera wosanditsata Ine, ndipo sanacita malamulo anga, Ndipo Samueli anakwiya; nalira kwa Yehova usiku wonse.
12 Ndipo Samueli analawirira m'mawa kuti akakomane ndi Sauli; ndipo munthu anamuuza Samueli kuti, Sauli anafika ku Karimeli, ndipo taonani, anaimika cikumbutso cace, nazungulira, napitirira, natsikira ku Giligala.
13 Ndipo Samueli anadza kwa Sauli; ndipo Sauli anati kwa iye, Yehova akudalitseni; ine ndinacita lamulo la Yehova.
14 Ndipo Samueli anati, Koma tsono kulirako kwa nkhosa ndirikumva m'makutu anga, ndi kulirako kwa ng'ombe ndirikumva, nciani?
15 Ndipo Sauli anati, Anazitenga kwa Aamaleki; pakuti anthu anasunga nkhosa zokometsetsa ndi ng'ombe, kuzipereka nsembe kwa Yehova Mulungu wanu; koma zina tinaziononga konse konse.
16 Pomwepo Samueli ananena ndi Sauli, Imani, ndidzakudziwitsani cimene Yehova wanena ndi ine usiku walero. Ndipo iyeyo anati kwa iye, Nenani.
17 Nati Samueli, M'mene munali wamng'ono m'maso a inu nokha, kodi simunaikidwa mutu wa mafuko a Israyeli? Ndipo Yehova anakudzozani mfumu ya Israyeli,
18 Ndipo Yehova anakutumani ulendo, kuti, Muka, nuononge konse konse Aamaleki akucita zoipawo, nuponyane nao kufikira utawatha.
19 Cifukwa ninji tsono simunamvera mau a Yehova, koma munathamangira zowawanya, ndi kucita coipa pamaso pa Yehova?
20 Ndipo Sauli ananena ndi Samueli, Koma ndinamvera mau a Yehova, ndipo ndinayenda njira Yehova anandituma ine, ndipo ndinabwera naye Agagi mfumu ya Amaleki, ndi Aamaleki ndinawaononga konse konse.
21 Koma anthuwo anatengako zowawanya, nkhosa ndi ng'ombe, zoposa za zija tidayenera kuziononga, kuziphera nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ku Giligala.
22 Ndipo Samueli anati, Kodi Yehova akondwera ndi nsembe zopsereza ndi nsembe zophera, monga ndi kumvera mau a Yehova? Taonani, kumvera ndiko kokoma koposa nsembe, kuchera khutu koposa mafuta a nkhosa zamphongo,
23 Pakuti kupanduka kuli ngati coipa ca kucita nyanga, ndi mtima waliuma uli ngati kupembedza milungu yacabe ndi maula. Popeza inu munakaniza mau a Yehova, Iyenso anakaniza inu, kuti simudzakhalanso mfumu.
24 Ndipo Sauli anati kwa Samueli, Ndinacimwa; pakuti ndinalumpha lamulo la Yehova, ndi mau anu omwe; cifukwa ndinaopa anthuwo, ndi kumvera mau ao.
25 Cifukwa cace tsono, mukhululukire cimo langa, nimubwerere pamodzi ndi ine, kuti ndikalambire Yehova.
26 Ndipo Samueli ananena ndi Sauli, Ine sindibwerera nanu; pakuti munakaniza mau a Yehova, ndipo Yehova anakaniza inu, kuti simudzakhalanso mfumu ya Israyeli.
27 Ndipo pakupotoloka Samueli kuti acoke, iye anagwira cilezi ca mwinjiro wace, ndipo cinang'ambika.
28 Ndipo Samueli ananena naye, Yehova anang'amba ufumu wa Israyeli lero kuucotsa kwa inu, naupatsa kwa mnansi wanu wina wabwino woposa inu.
29 Ndiponso Wamphamvu wa Israyeli sanama kapena kulapa; popeza iye sali munthu kuti akalapa.
30 Pomwepo iye anati, Ndinacimwa, koma mundicitire ulemu tsopano pamaso pa akuru a anthu anga, ndi pamaso pa Israyeli, nimubwerere pamodzi ndi ine, kuti ndikalambire Yehova Mulungu wanu.
31 Comweco Samueli anabwerera natsata Sauli; ndi Sauli analambira Yehova.
32 Ndipo Samueli anati, Bwerani naye kwa ine kuno Agagi mfumu ya Aamaleki. Ndipo Agagi anabwera kwa iye mokondwera. Nati Agagi, Zoonadi kuwawa kwa imfa kunapitirira.
33 Ndipo Samueli anati, Monga lupanga lako linacititsa akazi ufedwa, momwemo mai wako adzakhala mfedwa mwa akazi. Ndipo Samueli anamdula Agagi nthuli nthuli pamaso pa Yehova ku Giligala.
34 Pamenepo Samueli ananka ku Rama; ndi Sauli anakwera kunka ku nyumba yace ku Gibeya wa Sauli.
35 Ndipo Samueli sanadzanso kudzaona Sauli kufikira tsiku la imfa yace; koma Samueli analira cifukwa ca Sauli; ndipo Yehova anali ndi cisoni kuti anamlonga Sauli mfumu ya Israyeli.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Samueli, Iwe ukuti ulire cifukwa ca Sauli nthawi yotani, popeza Ine ndinamkana kuti asakhale mfumu ya Israyeli? Dzaza nyanga yako ndi mafuta, numuke, ndidzakutumiza kwa Jese wa ku Betelehemu; pakuti ndinadzionera mfumu pakati pa ana ace.
2 Ndipo Samueli anati, Ndikamuka bwanji? Sauli akacimva, adzandipha. Ndipo Yehova anati, Umuke nayo ng'ombe yaikazi, nunene kuti, Ndadza kudzaphera nsembe kwa Yehova.
3 Ndipo uitane Jese abwere kunsembeko, ndipo Ine ndidzakusonyeza cimene uyenera kucita; ndipo udzandidzozera iye amene ndidzakuchulira dzina lace.
4 Ndipo Samueli anacita cimene Yehova ananena, nadza ku Betelehemu. Ndipo akuru a mudziwo anadza kukomana naye monthunthumira, nati, Mubwera ndi mtendere kodi?
5 Nati iye, Ndi mtendere umene; ndadza kudzaphera nsembe kwa Yehova; mudzipatule ndi kufika ndi ine kunsembeko. Ndipo iye anapatula Jese ndi ana ace, nawaitanira kunsembeko.
6 Ndipo kunali, pakufika iwo, iye anayang'ana pa Eliyabu, nati, Zoonadi, wodzozedwa wa Yehova ali pamaso pace.
7 Koma Yehova ananena ndi Samueli, Vsayang'ane nkhope yace, kapena kutalika kwa msinkhu wace, popeza Ine ndinamkana iye; pakuti Yehova saona monga aona munthu; pakuti munthu ayang'ana cooneka ndi maso, koma Yehova ayang'ana mumtima.
8 Pamenepo Jese anaitana Abinadabu nampititsa pa Samueli. Ndipo iye adati, Koma uyunso Yehova sadamsankha.
9 Pamenepo Jese anapititsapo Sama. Ndipo anati, Koma uyunso Yehova sanamsankha.
10 Ndipo Jese anapititsapo ana ace amuna asanu ndi awiri. Koma Samueli anati kwa Jese, Yehova sanawasankha awa.
11 Ndipo Samueli anati kwa Jese, Ana anu ndi omwewa kodi? Nati iye, Watsala wina, mng'ono wa onse, ndipo taonani, iye alikuweta nkhosa. Ndipo Samueli anati kwa Jese, Tumiza munthu akamtenge; pakuti ife sitidzakhala pansi kufikira iye atadza kuno.
12 Ndipo anatumiza munthu, nabwera naye. Tsono iye anali wofiirira, ndi wa nkhope yokongola, ndi maonekedwe okoma. Ndipo Yehova anati, Nyamuka umdzoze, pakuti ndi ameneyu.
13 Pamenepo Samueli anatenga nyanga ya mafuta, namdzoza pakati pa abale ace; ndipo mzimu wa Yehova unalimbika pa Davide kuyambira tsiku lomweli. Ndipo Samueli ananyamuka, Danks ku Rama.
14 Koma mzimu wa Yehova unamcokera Sauli, ndi mzimu woipa wocokera kwa Yehova unambvuta iye.
15 Ndipo anyamata a Sauli ananena naye, Onani tsopano, mzimu woipa wocokera kwa Mulungu ulikubvuta inu.
16 Tsono inu mbuye wathu muuze anyamata anu, amene ali pamaso panu, kuti afune munthu wanthetemya wodziwa kuyimba zeze; ndipo kudzakhala, pamene mzimu woipa wocokera kwa Mulungu uli pa inu, iyeyo adzayimba ndi dzanja lace, ndipo mudzakhala wolama.
17 Ndipo Sauli anati kwa anyamata ace, Mundifunire tsono munthu wakudziwa kuyimba bwino, nimubwere naye kwa ine.
18 Ndipo mnyamata wace wina anayankha, nati, Taonani, ine ndaona mwana wa Jese wa ku Betelehemu, ndiye wanthetemya wodziwa kuyimbira, ndipo ali wa mtima wolimba ndi woyenera nkhondo, ndiponso ali wocenjera manenedwe ace; ndiye munthu wokongola, ndipo Yehova ali naye.
19 Cifukwa cace Sauli anatumiza mithenga kwa Jese, nati, Vnditumizire Davide, mwana wako, amene ali kunkhosa.
20 Ndipo Jese anatenga buru namsenza mkate, ndi thumba la vinyo, ndi: mwana wa mbuzi, nazitumiza kwa Sauli ndi Davide mwana wace.
21 Ndipo Davide anafika kwa Sauli, naima pamaso pace; ndipo iye anamkonda kwambiri, namsandutsa wonyamula zida zace.
22 Ndipo Sauli anatumiza kwa Jese, nati, Ulole kuti Davide aime pamaso panga; pakuti ndamkomera mtima.
23 Ndipo kunali kuti pamene mzimu woipawo wocokera kwa Mulungu unali pa Sauli, Davide anatenga zeze, naliza ndi dzanja lace; comweco Sauli anatsitsimuka, nakhala bwino, ndi mzimu woipa unamcokeraiye.
1 Pamenepo Afilisti anasonkhanitsa makamu ao a nkhondo, naunjikana ku Soko wa ku Yuda, namanga zithando pakati pa Soko ndi Azeka ku Efesi-damimu.
2 Ndipo Sauli ndi anthu a Israyeli anasonkhana, namanga zithando pa cigwa ca Ela, nandandalitsa nkhondo yao kuti akaponyane ndi Afilisti.
3 Ndipo Afilisti anaima paphiri tsidya lija, ndi Aisrayeli anaima paphiri tsidya lina; ndi pakati pao panali cigwa.
4 Ndipo ku zithando za Afilisti kunaturuka ciwinda, dzina lace Goliate wa ku Gati, kutalika kwace ndiko mikono isanu ndi umodzi ndi cikhato.
5 Ndipo anali ndi cisoti camkuwa pamutu pace, nabvala maraya aunyolo, olemera ngati masekeli zikwi zisanu za mkuwa,
6 nakuta msongolo wace ndi cobvala camkuwa, ndiponso pacikota pace panali nthungo yamkuwa.
7 Ndipo mtengo wa mkondo wace unali ngati mtanda woombera nsaru; ndi khali la mkondowo linalemera ngati masekeli mazana asanu ndi limodzi a citsulo; ndipo womnyamulira cikopa anamtsogolera.
8 Naima iye naitana makamu a nkhondo a Israyeli, nanena nao, Munaturukiranji kundandalitsa nkhondo yanu? Sindine Mfilisti kodi, ndi inu anyamata a Sauli? mudzisankhire munthu, atsikire kwa ine.
9 Akakhoza iyeyo kuponyana ndi ine ndi kundipha, tidzakhala ife akapolo anu; koma ine ndikamlaka, ndi kumupha, tsono mudzakhala inu akapolo athu, ndi kutitumikira ife.
10 Nati Mfilistiyo, Ine ndinyoza makamu a nkhondo a Israyeli lero; mundipatse munthu, kuti tilimbane ife awiri.
11 Ndipo pamene Sauli ndi Aisrayeli onse anamva mau ao a Mfilistiyo, anadodoma, naopa kwambiri.
12 Tsono Davide anali mwana wa M-efrati uja wa ku Betelehemu-Yuda, dzina lace ndiye Jese; ameneyu anali nao ana amuna asanu ndi atatu; ndipo m'masiku a Sauli munthuyo anali nkhalamba, mwa anthu.
13 Ndipo ana atatu akuru a Jese anatsata Sauli kunkhondoko; ndi maina ao a ana ace atatuwo adapita ku nkhondowo ndiwo Eliabu woyambayo, ndi mnzace womponda pamutu pace Abinadabu, ndi wacitatu Sama.
14 Ndipo Davide anali wotsiriza; ndi akuru atatuwo anamtsata Sauli.
15 Koma Davide akamuka kwa Sauli, nabwerera kudzadyetsa nkhosa za atate wace ku Betelehemu.
16 Ndipo Mfilistiyo anayandikira m'mawa ndi madzulo, nadzionetsera masiku makumi anai.
17 Ndipo Jese anati kwa Davide mwana wace, Uwatengere abale ako efa watirigu uyu wokazinga, ndi mikate iyi khumi, nuthamangire nazo kuzithando kwa abale ako;
18 nunyamule ncinci izi khumi zamase ukapatse mtsogoleri wa cikwi cao, nukaone m'mene akhalira abale ako, nulandire cikole cao,
19 Tsono Sauli, ndi iwowa, ndi anthu onse a Israyeli, anali m'cigwa ca Ela, ku nkhondo ya Afilisti.
20 Ndipo Davide anauka m'mamawa, nasiyira nkhosa wozisungira, nasenza zija, namuka, monga anamuuza Jese; ndipo iye anafika ku linga la magareta, napeza khamu lirikuturuka kunka poponyanira nkhondo lirikupfuula.
21 Ndipo Israyeli ndi Afilisti anandandalitsa nkhondo zao, khamu tina kuyang'anana ndi khamu lina.
22 Ndipo Davide anasiya akatundu ace m'dzanja la wosungira akatundu, nathamangira ku khamulo, nadza nalankhula abale ace.
23 Ndipo m'mene iye anali cilankhulire nao, onani cinakwerako ciwindaco, Mfilisti wa ku Gati, dzina lace ndiye Goliate, woturuka pakati pa mipambo ya Afilisti, nalankhula monga mau omwe aja; ndipo Davide anawamva.
24 Ndipo Aisrayeli onse, pakumuona munthuyo, anamthawa, naopa kwambiri.
25 Nati Aisrayeli, Kodi mwaona munthu uyu amene anakwera kuno? zoonadi iye anakwera kuti adzanyoze Israyeli, ndipo munthu wakumupha iye, mfumu idzamlemeza ndi cuma cambiri, nidzampatsa mwana wace wamkazi, nidzayesa nyumba ya atate wace yaufulu m'Israyeli.
26 Ndipo Davide analankhula ndi anthu akuima pafupi ndi iye, nati, Adzamcitira ciani munthu wakupha Mfilisti uyu, ndi kucotsa tonzo lace pakati pa Israyeli? pakuti Mfilisti uyu wosadulidwa ndiye yani, kuti azinyoza makamu a Mulungu wamoyo?
27 Ndipo anthuwo anamyankha motero, nati, Adzamcitira munthu wakumupha iye mwakuti mwakuti.
28 Ndipo Eliabu mkuru wace anamumva iye alikulankhula ndi anthu; ndipo Eliabu anapsa mtima ndi Davide, nati, Unatsikiranji kuno? ndi nkhosa zija zowerengeka unazisiya ndi yani, m'cipululu muja? Ine ndidziwa kudzikuza kwako ndi kuipa kwa mtima wako; pakuti watsika kuti udzaone nkhondoyi.
29 Ndipo Davide anati, Ndacitanji tsopano? Palibe cifukwa kodi?
30 Napotolokera iye kwa munthu wina, nalankhula mau omwewo; ndipo anthu anamyankhanso monga momwemo.
31 Ndipo pamene mau adanena Davide anamveka, anawapitiriza kwa Sauli; ndipo iye anamuitana.
32 Ndipo Davide anati kwa Sauli, Asade nkhawa munthu ali yense cifukwa ca iyeyo; ine kapolo wanu ndidzapita kuponyana ndi Mfilisti uyu.
33 Ndipo Sauli anati kwa Davide, Sukhoza iwe kukomana ndi Mfilisti uyu kukaponyana naye; pakuti iwe ndiwe mnyamata, koma iye anazolowera nkhondo kuyambira ubwana wace.
34 Ndipo Davide anati kwa Sauli, Ine kapolo wanu ndinalikusunga nkhosa za atate wanga; ndipo pakubwera mkango, mwina cimbalangondo ndi kutenga nkhosa ya gululo,
35 ndinacithamangira, ndi kucikantha, ndi kuiturutsa m'kamwa mwace; ndipo pamene cinaneliukira, ndinagwira cowa lace ndi kucikantha ndi kucipha.
36 Ine kapolo wanu ndinapha mkango ndi cimbalangondo zonse ziwiri; ndipo Mfilisti uyu wosadulidwa adzakhala ngati mmodzi wa izo, popeza wanyoza makamu a Mulungu wamoyo.
37 Nati Davide, Yehova wakundipulumutsa pa mphamvu ya mkango, ndi mphamvu ya cimbalangondo, Iyeyu adzandipulumutsa m'dzanja la Mfilisti uyu, Ndipo Sauli anati kwa Davide, Muka, Yehova akhale nawe.
38 Ndipo Sauli anabveka Davide zobvala zace za iye yekha, nambveka cisoti camkuwa pamutu pace, nambvekanso maraya aunyolo.
39 Ndipo Davide anamanga lupanga lace pamwamba pa zobvala zace, nayesa kuyenda nazo; popeza sanaziyesera kale. Ndipo Davide anati kwa Sauli, Sindikhoza kuyenda ndi izi; pakuti sindinazizolowera. Nazibvula Davide.
40 Natenga ndodo yace m'dzanja lace nadzisankhira miyala isanu yosalala ya mumtsinje, naiika m'thumba la kubusa, limene anali nalo ndilo cibete; ndi coponyera miyala cinali m'dzanja lace, momwemo anayandikira kwa Mfilistiyo.
41 Ndipo Mfilistiyo anadza, nayandikira kwa Davide; ndi wonyamula cikopa cace anamtsogolera.
42 Ndipo Mfilisti pakumwazamwaza maso, ndi kuona Davide, anampeputsa; popeza anali mnyamata cabe, wofiirira, ndi wa nkhope yokongola.
43 Ndipo Mfilisti anati kwa Davide, Ine ndine garu kodi, kuti iwe ukudza kwa ine ndi ndodo? Ndi Mfilistiyo anatukwana Davide nachula milungu yace.
44 Ndipo Mfilistiyo anati kwa Davide, Idza kuno kwa ine, ndidzapatsa mnofu wako kwa mbalame za mlengalenga, ndi kwa zirombo za kuthengo.
45 Ndipo Davide anati kwa Mfilistiyo, Iwe ukudza kwa ine ndi lupanga, ndi mkondo, ndi nthungo; koma ine ndafika kwa iwe m'dzina la Yehova wa makamu, Mulungu wa ankhondo a Israyeli amene iwe unawanyoza.
46 Lero lino Yehova adzakupereka iwe m'dzanja langa, ndipo ndidzakukantha, ndi kukucotsera mutu wako. Ndipo lero ndidzapatsa mitembo ya makamu a Afilisti kwa mbalame za mlengalenga, ndi kwa zirombo za dziko lapansi; kuti dziko lonse likazindikire kuti kwa Israyeli kuli Mulungu.
47 Ndi msonkhano wonse uno udzazindikira kuti Yehova sapulumutsa ndi lupanga, kapena ndi mkondo; pakuti Yehova ndiye mwini nkhondo, ndipo iye adzakuperekani inu m'manja athu.
48 Ndipo kunali, pamene Mfilistiyo anadzikonza, nadza, nasendera pafupi kuti akomane ndi Davide, Davide anafulumira, nathamangira ku khamulo, kuti akomane ndi Mfilistiyo.
49 Ndipo Davide anapisa dzanja lace m'thumba mwace, naturutsamo mwala, nauponya, nalasa Mfilistiyo pamphumi; ndi mwalawo unalowa m'mphumi, ndipo iye anagwa pansi cafufumimba.
50 Comweco Davide anapambana Mfilistiyo ndi mwala wa coponyera cace, nakantha Mfilistiyo, namupha. Koma m'dzanja la Davide munalibe lupanga.
51 Potero Davide anathamanga naima pa Mfilistiyo, nagwira lupanga lace, nalisolola m'cimace, namtsiriza nadula nalo mutu wace. Ndipo pakuona Afilisti kuti ciwinda cao cidafa, anathawa.
52 Ndipo anthu a Israyeli ndi Ayuda ananyamuka, napfuula, nathamangira Afilistiwo, mpaka ufika kucigwako, ndi ku zipata za Ekroni. Ndipo Afilistiwo olasidwa anagwa pa njira ya ku Saraimu, kufikira ku Gad ndi ku Ekroni.
53 Ndipo ana a Israyeli atathamangira Afilisti, anabwerera nafunkha za m'zithando zao.
54 Ndipo Davide anatenga mutu wa Mfilistiyo, napita nao ku Yerusalemu; koma zida zace anazisunga m'hema wace.
55 Ndipo pamene Sauli anaona Davide alikuturukira kwa Mfilistiyo, iye anati kwa Abineri, kazembe wa khamu la nkhondo, Abineri, mnyamata uyu ndi mwana wa yani? Nati Abineri, Pali moyo wanu, mfumu, ngati ndidziwa.
56 Ndipo mfumu inati, Ufunsire kuti mnyamatayo ndi mwana wa yani.
57 Ndipo pamene Davide anabwera, atapha Mfilistiyo, Abineri anamtenga, nafika naye pamaso pa Sauli, mutu wa Mfilistiyo uli m'dzanja lace.
58 Ndipo Sauli anati kwa iye, Mnyamata iwe, ndiwe mwana wa yani? Davide nayankha, Ndiri mwana wa kapolo wanu Jese wa ku Betelehemu.
1 Ndipo kunali, pakutsiriza iye kulankhula ndi Sauli, mtima wa Jonatani unalumikizika ndi mtima wa Davide, ndipo Jonatani anamkonda iye monga moyo wa iye yekha.
2 Ndipo Sauli anamtenga tsiku lomwelo, osamlolanso apite kwao kwa atate wace.
3 Pamenepo Jonatani ndi Davide anapangana pangano, pakuti adamkonda iye ngati moyo wa iye yekha.
4 Ndipo Jonatani anabvula maraya ace anali nao, napatsa Davide, ndi zobvala zace, ngakhale lupanga lace, ndi uta wace, ndi lamba lace.
5 Ndipo Davide anaturuka kunka kuli konse Sauli anamtumako, nakhala wocenjera; ndipo Sauli anamuika akhale woyang'anira anthu a nkhondo; ndipo ici cinakomera anthu onse, ndi anyamata a Sauli omwe.
6 Ndipo kunali pakudza iwo, pamene Davide anabwera atapha Afilistiwo, anthu akazi anaturuka m'midzi yonse ya Israyeli, ndi kuyimba ndi kubvina, kuti akakomane ndi mfumu Sauli, ndi malingaka, ndi cimwemwe, ndi zoyimbira.
7 Ndipo akazi anathirirana mang'ombe m'kuyimba kwao, nati, Sauli anapha zikwi zace, Koma Davide zikwi zace zankhani.
8 Koma Sauli anakwiya ndithu, ndi kunenaku kunamuipira; nati, Kwa Davide anawereogera zikwi zankhani, koma kwa ine zikwi zokha; cimperewera ncianioso, koma ufumu wokha?
9 Ndipo kuyambira tsiku lomwelo ndi m'tsogolo mwace, Sauli anakhala maso pa Davide.
10 Ndipo kunali m'mawa mwace, mzimu woipa wocokera kwa Mulungu unamgwira Sauli mwamphamvu, iye nalankhula moyaruka m'nyumba yace; koma Davide anayimba ndi dzanja lace, monga amacita tsiku ndi tsiku; koma m'dzanja la Sauli munali mkondo.
11 Ndipo Sauli anaponya mkondowo; pakuti anati, Ndidzapyoza Davide ndi kumphatikiza ndi khoma. Ndipo Davide analewa kawiri kucoka pamaso pace.
12 Ndipo Sauli anaopa Davide, cifukwa Yehova anali naye, koma adamcokera Sauli.
13 Cifukwa cace Sauli anamcotsa kuti asakhale naye, namuika akhale mtsogoleri wace wa anthu cikwi cimodzi; ndipo iye anatsogolera anthu kuturuka ndi kubwera nao.
14 Ndipo Davide anakhala wocenjera m'mayendedwe ace onse; ndipo Yehova anali naye.
15 Ndipo pamene Sauli anaona kuti analikukhala wocenjera ndithu anamuopa.
16 Koma Aisrayeli onse ndi Ayuda onse anamkonda Davide pakuti anawatsogolera kuturuka ndi kulowa nao.
17 Ndipo Sauli anati kwa Davide, Ona, mwana wanga wamkazi wamkuru, dzina lace Merabi, iyeyo ndidzakupatsa akhale mkazi wako; koma undikhalire ngwazi, nuponye nkhondo za Yehova. Pakuti Sauli anati, Dzanja langa lisamkhudze, koma dzanja la Afilisti ndilo.
18 Ndipo Davide anati kwa Sauli, Ine ndine yani, ndi moyo wanga uli wotani, kapena banja la atate wanga liri lotani m'Israyeli, kuti ine ndidzakhala mkamwini wa mfumu?
19 Koma kunali nthawi imene akadapatsa Merabi mwana wamkazi wa Sauli kwa Davide, iye anapatsidwa kwa Adrieli Mholati kukhala mkazi wace.
20 Ndipo Mikala mwana wamkazi wa Sauli anakonda Davide; ndipo pakumva Sauli, anakondwera nako.
21 Nati Sauli, Ndidzampatsa iye, kuti amkhalire msampha, ndi kuti dzanja la Afilisti limgwere. Cifukwa cace Sauli ananena ndi Davide, Lero udzakhala mkamwini wanga kaciwiri.
22 Ndipo Sauli analamulira anyamata ace, nati, Mulankhule naye Davide m'tseri, ndi kuti, Taonani mfumu akondwera nanu, ndi anyamata ace onse akukondani; cifukwa cace tsono, khalani mkamwini wa mfumu.
23 Ndipo anyamata a Sauli analankhula mau awa m'makutu a Davide. Nati Davide, Kodi muciyesera cinthu copepuka kukhala mkamwini wa mfumu, popeza ndiri munthu wosauka, ndi wopeputsidwa.
24 Ndipo anyamata a Sauli anamuuza, kuti, Anatero Davide.
25 Nati Sauli, Mudzatero kwa Davide, kuti mfumu safuna colowolera cina, koma nsonga za makungu zana limodzi za Afilisti, kuti abwezere cilango adani a mfumu. Koma Sauli anaganizira kupha Davide ndi dzanja la Afilisti.
26 Ndipo pamene anyamata ace anauza Davide mau awa, kudamkomera Davide kukhala mkamwini wa mfumu.
27 Ndipo asanathe masikuwo, ananyamuka Davide, ndi anthu ace, nakaphako Afilisti mazana awiri, ndipo Davide anatenga nsonga za makungu ao nazipatsa mofikira kwa mfumu, kuti akhale mkamwini wa mfumu. Ndipo Sauli anampatsa Mikala mwana wace wamkazi akhale mkazi wace.
28 Ndipo Sauli anaona, nadziwa kuti Yehova ali ndi Davide; ndi kuti Mikala mwana wa Sauli anamkonda Davide.
29 Sauli nayamba kumuopa Davide kopambana; ndi Sauli anali mdani wa Davide masiku onse.
30 Pomwepo mafumu a Afilisti anaturuka; ndipo nthawi zonse anaturuka iwo, Davide anali wocenjera koposa anyamata onse a Sauli, comweco dzina lace linatamidwa kwambiri.
1 Ndipo Sauli analankhula kwa Jonatani mwana wace, ndi anyamata ace onse kuti amuphe Davide.
2 Koma Jonatani mwana wa Sauli anakondwera kwambiri ndi Davide. Ndipo Jonatani anauza Davide, nati, Sauli atate wanga alikufuna kukupha; cifukwa cace tsono ucenjere m'mawa, mukhale m'malo mosadziwika, nubisale;
3 ndipo ine ndidzaturuka ndi kuima pa mbali ya atate wanga kumunda kumene kuli iwe, ndipo ndidzalankhula ndi atate wanga za iwe; ndipo ndikaona kanthu ndidzakudziwitsa.
4 Ndipo Jonatani analankhula ndi atate wace mobvomereza Davide, nanena naye, Mfumu asacimwire mnyamata wace Davide; cifukwa iyeyo sanacimwira inu, ndipo nchito zace anakucitirani zinali zabwino ndithu;
5 popeza iye anataya moyo wace nakantha Mfilistiyo, ndipo Yehova anacitira Aisrayeli onse cipulumutso cacikuru, inu munaciona, nimnnakondwera; tsono mudzacimwiranji mwazi wosalakwa, ndi kumupha Davide popanda cifukwa?
6 Ndipo Sauli anamvera mau a Jonatani; nalumbira, Pali Yehova, sadzaphedwa iye.
7 Pamenepo Jonatani anaitana Davide, namuuza zonsezi. Ndipo Jonatani anafika naye Davide kwa Sauli, iye nakhalanso pamaso pace monga kale.
8 Ndipo kunalinso nkhondo; ndipo Davide anaturuka, nakamenyana ndi Afilisti, nawapha ndi maphedwe akuru, ndipo iwo anamthawa iye.
9 Ndipo mzimu woipa wocokera kwa Yehova unali pa Sauli, pakukhala iye m'nyumba mwace, ndi mkondo wace m'dzanja lace; ndipo Davide anayimba ndi dzanja lace.
10 Ndipo Sauli anayesa kupyoza Davide kumphatikiza kukhoma ndi mkondowo; koma iye anadzilanditsa kucoka pamaso pa Sauli; ndipo analasa khoma; ndipo Davide anathawa napulumuka usiku uja.
11 Ndipo Sauli anatumiza mithenga ku nyumba ya Davide imdikire, ndi kumupha m'mawa; koma Mikala mkazi wa Davide anamuuza, nati, Ukapanda kupulumutsa moyo wako usiku uno, udzaphedwa ndithu m'mawa.
12 Comweco Mikala anamtsitsira Davide pazenera, namuka iye, nathawa, napulumuka.
13 Ndipo Mikala anatenga cifanizo naciika pakama, naika mtsamiro wa ubweya wa mbuzi kumutu kwace, nacipfunda zopfunda.
14 Ndipo pamene Sauli anatumiza mithenga kuti ikamgwire Davide, anati, iye alikudwala.
15 Ndipo Sauli anatumiza mithengayo kuti ikaone Davide, nati, Mumtengere iye pa kama wace, kuti ndidzamuphe.
16 Ndipopakulowamithengayo, onani, pakama pali cifanizo ndi mtsamiro wa ubweya wa mbuzi kumutu kwace.
17 Nati Sauli kwa Mikala, Wandinyengeranii comweci, ndi kulola mdani wanga apulumuke? Ndipo Mikala anayankha Sauli, iye anati kwa ine, Undilole ndipite, ndingakuphe.
18 Comweco anathawa Davide, napulumuka, nafika kwa Samueli: ku Rama, namuuza zonse Sauli anamcitira. Ndipo iye ndi Samueli anakhala ku Nayoti.
19 Ndipo wina anauza Sauli, kuti, Onani Davide ali ku Nayoti m'Rama.
20 Ndipo Sauli anatumiza mithenga kuti igwire Davide, ndipo pamene inaona gulu la aneneri alikunenera, ndi Samueli mkuru wao alikuimapo, mzimu wa Mulungu unagwera-mithenga ya Sauli, ninenera iyonso.
21 Ndipo pamene anauza Sauli, iye anatumiza mithenga yina; koma iyonso inanenera. Ndipo Sauli anatumiza mithenga kacitatu, nayonso inanenera.
22 Pamenepo iyenso anamuka ku Rama, nafika ku citsime cacikuru ciri ku Seku, nafunsa Dati, Samueli ndi Davide ali kuti? Ndipo wina anati, Taonani, ali ku Nayoti m'Rama.
23 Ndipo anapita komweko ku Nayoti m'Rama; ndi mzimu wa Mulungu unamgwera iyenso; ndipo anapitirira, nanenera, mpaka anafika ku Nayoti m'Rama.
24 Ndiponso anabvula zobvala zace, naneneranso pamaso pa Samueli nagona wamarisece usana womwe wonse, ndi usiku womwe wonse. Cifukwa cace amati, Kodi Saulinso ali pakati pa aneneri?
1 Ndipo Davide anathawa ku Nayoti m'Rama, nadzanena pamaso pa Jonatani, Ndacitanji ine? kuipa kwanga kuli kotani? ndi chimo langa la pamaso pa atate wanu ndi ciani, kuti amafuna moyo wanga?
2 Namyankha, Usatero iai, sudzafa; ona, atate, wanga sacita kanthu kakakuru kapena kakang'ono wosandidziwitsa ine; atate wanga adzandibisiranji cinthu cimeneci? Si kutero ai.
3 Ndipo Davide analumbiranso nati, Atate wako adziwatu kuti wandikomera mtima; nati, Jonatani asadziwe ici, kuti angamve cisoni; koma pali Yehova, ndiponso pali moyo wako, pakati pa ine ndi imfa pali ngati phazilimodzi.
4 Ndipo Jonatani anati kwa Davide, Ciri conse mtima wako unena, ndidzakucitira.
5 Nati Davide kwa Jonatani, Onani, mawa mwezi ukhala, ndipo ine ndiyenera kupita kukadya kwa mfumu, wosatsala; koma undilole ndikabisale kuthengo, kufikira tsiku lacitatu madzulo ace.
6 Atate wako akandifuna pang'ono ponse, unene kuti, Davide anandiumirira ndimlole athamangire kwao ku Betelehemu, pakuti kumeneko kuli nsembe ya pacaka ya banja lao lonse.
7 Tsono akati, Cabwino; kapolo wako adzakhala ndi mtendere; koma akapsa mtima, uzindikirepo kuti anatsimikiza mtima kundicitira coipa.
8 Cifukwa cace ucitire kapolo wako zokoma mtima; popeza wamcititsa kapolo wako kupangana nawe pangano la kwa Yehova; koma ngati mwa ine muli coipa ciri conse, undiphe wekha; udzapita nane bwanji kwa atate wako?
9 Ndipo Jonatani anati, lai ndi pang'ono ponse; ine ndikadziwa konse kuti atate wanga anatsimikiza mtima kukucitira coipa, sindidzadziwitsa iwe kodi?
10 Tsono Davide anati kwa Jonatani, Adzandiuza ndani ngati atate wako alankhulira iwe mokalipa?
11 Nati Jonatani kwa Davide, Tiyeni timuke kuthengo. Namuka onse awiri kuthengoko.
12 Ndipo Jonatani anati kwa Davide, Yehova, Mulungu wa Israyeli, akhale mboni; nditaphera mwambi atate wanga mawa dzuwa lino, kapena mkuca, onani, pakakhala kanthu kabwino kakucitira Davide, sindidzakutumira mthenga ndi kukuululira kodi?
13 Mulungu alange Jonatani, ndi kuonjezapo, ngati atate wanga akondwera kukucitira coipa, ine osakuululira, ndi kukucotsa kuti upite mumtendere; ndipo Yehova akhale nawe, monga anakhala naye atate wanga.
14 Ndipo undionetsere cifundo ca Yehova, si pokhala ine ndi moyo pokha, kuti ndingafe;
15 komanso usaleke kucitira cifundo a m'nyumba yanga nthawi zonse; mungakhale m'tsogolomo Yehova atathera adani onse a Da vide pa dziko lapansi.
16 Comweco Jonatani anapangana pangano ndi nyumba ya Davide, ndipo Yehova anakwaniritsa izi polanga adani a Davide.
17 Ndipo Jonatani anamlumbiritsa Davide kaciwiri, cifukwa anamkonda; popeza anamkonda monga anakonda moyo wa iye yekha.
18 Tsono Jonatani ananena kwa Davide, Mawa mwezi ukhala; ndipo adzakufuna, popeza udzasoweka pamalo pako.
19 Ndipo atapita masiku atatu, utsike msanga, nufike kumene unabisala tsiku la mrandu uja, nukhale pa mwala wa Ezeri.
20 Ndipo ine ndidzaponya mibvi itatu pambali pace, monga ngati ndirikuponya pacandamali.
21 Ndipo taona, ndidzatumiza mnyamatayo, ndi kuti, Kafune mibviyo, Ndikamuuza mwanayo, kuti, Taona mibvi iri cakuno; uitole nubwere, popeza pali mtendere kwa iwe, palibe kanthu, pali Yehova.
22 Koma ndikati kwa mnyamatayo, Ona mibvi iri kutsogoloko; pamenepo unyamuke ulendo wako; popeza Yehova wakuuza umuke.
23 Ndipo za cija tinakambirana iwe ndi ine, taona, Yehova ali pakati pa ife nthawi zonse.
24 Comweco Davide anabisala kuthengo; ndipo pakukhala mwezi, mfumu inakhala pansi kudya.
25 Mfumu nikhala pa mpando wace, monga adafocita nthawi zina, pa mpando wa pafupi pa khoma. Ndipo Jonatani anaimirira, ndi Abineri anakhala pa mbali ya Sauli; koma Davide anasoweka pamalo pace.
26 Koma Sauli sananena kanthu tsiku lomwelo; cifukwa anaganizira, Kanthu kanamgwera iye, ali wodetsedwa; indedi ali wodetsedwa.
27 Ndipo kunali tsiku laciwiri mwezi utakhala, Davide adasowekanso pamalo pace; ndipo Sauli anati kwa Jonatani mwana wace, Mwana wa Jese walekeranji kubwera kudya dzulo ndi lero lomwe?
28 Ndipo Jonatani anayankha Sauli, Davide anandiumiriza ndimlole amuke ku Betelehemu;
29 nati, Ndiloleni, ndimuke; cifukwa banja lathu lipereka nsembe m'mudzimo; ndi mbale wanga anandiuzitsa ndifikeko; tsono ngati wandikomera mtima undilole ndicoke, ndikaone abale anga. Cifukwa ca ici safika ku gome la mfumu.
30 Pamenepo Sauli anapsa mtima ndi Jonatani, nanena naye, Iwe mwana wa mkazi wa matsutso ndi wopikisana, sindidziwa kodi kuti wasankha mwana wa Jeseyo kudzinyaza wekha, ndi usiwa wa mai wako yemwe?
31 Popeza nthawi yonse mwana wa Jeseyo akhala ndi moyo padziko, koma sudzakhazikika iwe, kapena ufumu wako. Cifukwa cace tumiza tsopano numtengere kuno kwa ine, popeza adzafa ndithu,
32 Ndipo Jonatani anayankha Sauli atate wace, nanena, Aphedwe cifukwa ninji? anacitanji?
33 Ndipo Sauli anamponyera mkondo kuti amgwaze; momwemo Jonatani anazindikira kuti atate wace anatsimikiza mtima kupha Davide.
34 Pamenepo Jonatani anauka pagome wolunda ndithu, osadya kanthu tsiku laciwiri la mwezi, pakuti mtima wace unali ndi cisoni cifukwa ca Davide, popeza atate wace anamcititsa manyazi.
35 Ndipo m'mawa, Jonatani ananka kuthengoko pa nthawi imene anapangana ndi Davide, ali ndi kamnayamata.
36 Ndipo anauza mnyamata waceyo, Thamanga uzikatola mibvi Imene ndidzaponya; ndipo analikuthamanga mnyamatayu, iye anaponya mubvi kuutumphitsa iye.
37 Ndipo mnyamatayo atafika pa malo a mubvi umene Jonatani anauponya, Jonatani anapfuulira mnyamatayo, nati, Mubviwo suli m'tsogolo mwako kodi?
38 Ndipo Jonatani anapfuulira mnyamatayo, nati, Yendesa, fulumira, usaima. Ndi mnyamata wa Jonatani anatola mibvi, nafika kwa mbuye wace.
39 Koma mnyamatayo sanadziwa kanthu; Davide ndi Jonatani okha anadziwa za mranduwoo.
40 Ndipo Jonatani anapatsa mnyamata wace zida zace, nanena naye, Muka, tenga izi kunka nazo kumudzi.
41 Pomwepo pocoka mnyamatayo, Davide anauka cakumwera, nagwa nkhope yace pansi, nawerama katatu; ndipo iwowa anapsompsonana, nalirirana, kufikira Davide analiritsa.
42 Ndipo Jonatani ananena kwa Davide, Muka mumtendere, popeza tonsefe tinalumbira m'dzina la Yehova, kuti, Yehova adzakhala pakati pa ine ndi iwe, ndi pakati pa mbeu yanga ndi mbeu yako, nthawi zamuyaya.
43 Ndipo iye ananyamuka nacoka; koma Jonatani anamuka kumudzi.
1 Ndipo Davide anafika ku Nobi kwa! Ahimeleki wansembeyo; ndipo Ahimeleki anadza kukomana ndi Davide alikunjenjemera, nanena naye, Muli nokha bwanji, palibe munthu wina nanu?
2 Nati Davide kwa Ahimeleki wansembeyo, Mfumu inandilamulira nchito, ninena nane, Asadziwe munthu ali yense kanthu za nchito imene ndakutumira ndi kukulamulira; ndipo ndawapanga anyamatawo ku malo akuti.
3 Cifukwa cace tsono muli ndi ciani? mundipatse m'dzanja langa mikate isanu, kapena ciri conse muli naco.
4 Ndipo wansembeyo anayankha Davide nati, Ndiribe mkate wacabe, koma ulipo mkate wopatulika; pokhapo ngati anyamatawo anadzisunga kupewa akazi.
5 Ndipo Davide anayankha wansembeyo, nati naye, Zoonadi tinafulatira akazi monga masiku atatu; cicokere ine, zotengera za anayamatawo zinali zopatulika ungakhale unali ulendo wacabe; koposa kotani nanga zotengera zao zikhala zoyera lero?
6 Comweco wansembeyo anampatsa mkate wopatulika, popeza panalibe mkate wina, koma mkate woonekera, umene adaucotsa pamaso pa Yehova, kuti akaike mkate wotentha tsiku lomwelo anacotsa winawo.
7 Tsono munthu wina wa anyamata a Sauli anali komweko, tsiku lija, anacedwetsedwa pamaso pa Yehova; dzina lace ndiye Doegi wa ku Edomu, kapitao wa abusa a Sauli.
8 Ndipo Davide ananena ndi Ahimeleki, Nanga pano m'dzanja mwanu mulibe mkondo kapena lupanga kodi? cifukwa ine sindinatenge lupanga langa kapena zida zanga, popeza mrandu wa mfumu ukuti ndifulumire.
9 Nati wansembeyo, Lupanga la Goliate Mfilisti munamuphayo m'cigwa ca Ela, onani-liripo lokulunga m'nsaru, kumbuyo kwa efodi; mukafuna kutenga limenelo, tengani; popeza pano palibe lina, Ndipo Davide anati, Palibe lina lotere longa lijalo, ndipatseni.
10 Ndipo Davide ananyamuka, nathawa tsiku lomwelo cifukwa ca kuopa Sauli, namuka kwa Akisi mfumu ya ku Gati.
11 Ndipo anyamata a Akisi ananena naye, Uyu si Davide mfumu ya dzikolo kodi? Sanathirirana mang'ombe za iye kodi m'magule ao, ndi kuti, Sauli anapha zikwi zace, Koma Davide zikwi zace zankhani?
12 Ndipo Davide anasunga mau awa mumtima mwace, naopa kwambiri Akisi mfumu ya Gati.
13 Nasanduliza makhalidwe ace pamaso pao, nadzionetsera m'manja mwao ngati wamisala, nangolembalemba pa zitseko za cipata, nakhetsa dobvu lace pa ndebvu yace.
14 Tsono Akisi ananena ndi anyamata ace, Taonani, mupenya kuti munthuyo ngwa misala; mwabwera naye kwa ine cifukwa ninji?
15 Kodi ndisowa anthu amisala kuti mwabwera ndi uyu kuti akhale wamisala pamaso panga? Kodi uyu adzalowa m'nyumba mwanga?
1 Motero Davide anacoka kumeneko, napulumukira ku phanga la ku Adulamu; ndipo pamene abale ace ndi banja lonse la atate wace anamva, iwo anatsikira kumeneko kwa iye.
2 Ndipo yense wosautsidwa, ndi yense wa ngongole, ndi yense wowawidwa mtima, anaunjikana kwa iye; iye nakhala mtsogoleri wao; ndipo anali nao anthu ngati mazana anai.
3 Ndipo Davide anacoka kumeneko kunka ku Mizipa wa ku Moabu; nati kwa mfumu ya Moabu, Mulole atate wanga ndi mai wanga aturuke nakhale nanu, kufikira ndidziwa cimene Mulungu adzandidtira.
4 Ndipo anawatenga kumka nao pamaso pa mfumu ya Moabu; ndipo iwo anakhala naye nthawi yonse Davide anali ku lingalo.
5 Ndipo mneneri Gadi anati kwa Davide, Musamakhala m'lingamo; cokani, mulowe m'dziko la Yuda. Potero Davide anacokako, nafika ku nkhalango ya Hereti.
6 Pakumva Sauli kuti anadziwika Davide, ndi anthu ace akukhala naye, Sauti analikukhala m'Gibeya, patsinde pa mtengo wa kumsanje, m'dzanja lace munali mkondo wace, ndi anyamata ace onse anaimirira pali iye.
7 Ndipo Sauli anati kwa anyamata ace akuima comzinga, Imvani tsopano, inu a Benjamini; kodi mwana wa Jese adzakupatsani inu nonse minda, ndi minda yamphesa, kodi adzakuikani mukhale atsogoleri a zikwi ndi a mazana;
8 kuti inu nonse munapangana dwembu pa ine, ndipo palibe wina wakundiululira kuti mwana wanga anapangana pangano ndi mwana wa Jese, ndipo palibe wilia wa inu wakundidtira cifundo kapena kundidziwitsa kuti mwana wanga anafulumiza mnyamata wanga kundilalira monga lero lomwe?
9 Pamenepo Doegi wa ku Edomu, anaimirira ndi anyamata a Sauli, nayankha, nati, Ine ndinamuona mwana wa Jeseyo alikufika ku Nobi, kwa Ahimeleki mwana wa Ahitubu.
10 Ndipo iye anamfunsira kwa Yehova, nampatsa cakudya, nampatsanso lupanga la Gotiate Mfilistiyo.
11 Pamenepo mfumu anatuma mthenga kukaitana Ahimeleki wansembeyo, mwana wa Ahitubu, ndi banja lonse la atate wace, ansembe a ku Nobi; ndipo iwo onse anafika kwa mfumu.
12 Ndipo Sauli anati, Imva tsopano iwe mwana wa Ahitubu. Nayankha iye, Ndine, mbuye wanga.
13 Ndipo Sauli anati kwa iye, Munapangana dwembu pa ine bwanji, iwe ndi mwana wa Jese, kuti unampatsa iye mkate, ndi lupanga, ndi kumfunsira kwa Mulungu kuti iye andiukire, kundilalira, monga lero lomwe?
14 Ndipo Ahimeleki anayankha mfumu, nati, Ndipo ndani mwa anyamata anu onse ali wokhulupirika ngati Davide amene, mkamwini wa mfumu; wakuyenda mu uphungu wanu, nalemekezeka m'nyumba mwanu?
15 Kodi ndayamba lero kumfunsira kwa Mulungu? Musatero iai; mfumu asanenera mnyamata wace kanthu, kapena nyumba yonse ya atate wanga; popeza ine mnyamata wanu sindidziwa kanthu ka izi zonse, ndi pang'ono ponse.
16 Ndipo mfumu inati, Ukufa ndithu Ahimeleki, iwe ndi banja lonse la atate wako.
17 Mfumu niuza asilikari akuima comzinga iye, Potolokani, iphani ansembe a Yehova; cifukwa agwirizana ndi Davide, ndipo anadziwa kuti alinkuthawa, koma sanandiululira. Koma anayamata a mfumu sanafuna kutambalitsa manja ao kupha ansembe a Yehova.
18 Pamenepo mfumu inati kwa Doegi, Potoloka iwe nuwaphe ansembewo. Ndipo Doegi wa ku Edomu anapotoloka, nagwera ansembewo, napha tsikulo makumi asanu ndi atatu mphambu asanu akubvala efodi wabafuta.
19 Ndipo anakantha Nobi ndiwo mudzi wa ansembe ndi lupanga lakuthwa, anthu amuna ndi akazi, ana ndi makanda, ng'ombe ndi aburu, ndi nkhosa, ndi lupanga lakuthwa.
20 Ndipo mmodzi wa ana a Ahimeleki, mwana wa Ahitubu, dzina lace ndiye Abyatara, anapulumuka, nathawira kwa Davide.
21 Ndipo Abyatara anadziwitsa Davide kuti Sauli anapha ansembe a Yehova.
22 Ndipo Davide anati kwa Abyatara, Tsiku lija Doegi wa ku Edomu anali kumeneko, ndinadziwiratu kuti adzauzadi Sauli; ine ndinafetsa anthu onse a nyumba ya atate wako.
23 Ukhale ndi ine, usaopa; popeza iye wakufuna moyo wanga afuna moyo wako; koma ndi ine udzakhala mosungika.
1 Tsono anauza Davide, kuti, Onani Afilisti alikuponyana ndi Keila, nafunkha za m'madwale.
2 Cifukwa cace Davide anafunsira kwa Yehova, nati, Ndimuke kodi kukakantha Afilisti aja? Ndipo Yehova anati kwa Davide, Muka, nukanthe Afilisti, ndi kupulumutsa Keila.
3 Ndipo anyamata a Davide ananena naye, Taonani, ife tikhalira m'mantha ku Yuda kuno; koposa kotani nanga tikafika ku Keila kuponyana ndi makamu a nkhondo a Afilisti.
4 Tsono Davide anafunsiranso kwa Yehova. Ndipo Yehova anamyankha iye, nati, Nyamuka, nutsikire ku Keila; pakuti ndidzapereka Afilisti m'dzanja lako.
5 Comweco Davide ndi anthu ace anamuka ku Keila, naponyana ndi Afilisti, natenga ng'ombe zao, nawapha ndi kuwapulula kwambiri Motero Davide analanditsa okhala m'Keila.
6 Ndipo kunali kuti Abyatara mwana wa Ahimeleki pakuthawira kwa Davide ku Keila, anatsika ali ndi efodi m'dzanja lace.
7 Ndipo anthu anauza Sauli kuti Davide wafika ku Keila. Ndipo Sauli anati, Mulungu wampereka m'dzanja langa; pakuti atsekerezeka, popeza analowa m'mudzi wa zitseko ndi mipiringidzo.
8 Ndipo Sauli anamemeza anthu onse kunkhondo, kuti atsikire ku Keila, kumangira misasa Davide ndi anthu ace.
9 Ndipo Davide anadziwa kuti Sauli analikulingalira zomcitira zoipa; nati kwa Abyatara wansembe, Bwera kuno ndi efodi.
10 Nati Davide, Yehova, Mulungu wa Israyeli, mnyamata wanu wamva zoona kuti Sauli afuna kudza ku Keila, kuononga mudziwo cifukwa ca ine.
11 Kodi amuna a ku Keila adzandipereka m'dzanja lace? Kodi Sauli adzatsikira ndithu, monga mnyamata wanu wamva? Yehova Mulungu wa Israyeli, ndikupemphani, muuze mnyamata wanu. Ndipo Yehova anati, Adzatsika.
12 Tsono Davide anati, Kodi amuna a ku Keila adzandipereka ine ndi anyamata anga m'dzanja la Sauli? Ndipo Yehova anati, Adzakupereka.
13 Potero Davide ndi anyamata ace, ndiwo monga ngati mazana asanu ndi limodzi, ananyamuka, naturuka ku Keila, nayendayenda kuli konse adakhoza kuyendako. Ndipo anauza Sauli kuti Davide wapulumuka ku Keila; iye naleka kumtsata.
14 Ndipo Davide anakhala m'cipululu m'ngaka, nakhala m'dziko la mapiri m'cipululu ca Zifi. Ndipo Sauli anamfunafuna masiku onse, koma Mulungu sadampereka m'dzanja lace.
15 Ndipo Davide anaona kuti Sauli adaturuka kudzafuna moyo wace; Davide nakhala m'cipululu ca Ziti m'nkhalango.
16 Ndipo Jonatani mwana wa Sauli ananyamuka, napita kwa Davide kunkhalangoko, namlimbitsa dzanja lace mwa Mulungu.
17 Ndipo iye ananena naye, Usaopa; cifukwa dzanja la Sauli atate wanga silidzakupeza; iwe udzakhala mfumu ya Israyeli, ndipo ine ndidzakhala wotsatana nawe, icinso Sauli atate wanga acidziwa.
18 Ndipo awiriwo anapangana pangano pamaso pa Yehova; ndipo Davide anakhala kunkhalango, koma Jonatani anapita ku nyumba yace.
19 Ndipo a ku Zifi anakwera kwa Sauli ku Gibeya, nati, Davide salikubisala kwathu kodi, m'ngaka za m'nkhalango, m'phiri la Hakila. Umene Uri kumwera kwa cipululu?
20 Cifukwa cace mfumu, tsikani, monga umo mukhumbire m'mtima mwanu kutsika; ndipo kudzakhala kwathu kumpereka iye m'dzanja la mfumu.
21 Sauli nati, Mudalitsike inu kwa Yehova; cifukwa munandicitira ine cifundo.
22 Mukanitu kuti mukadziwitse ndithu, ndi kudziwa ndi kuona mbuto m'mene akhalitsa, ndi amene adamuona m'menemo; cifukwa anandiuza kuti iye acita mocenjera ndithu.
23 Cifukwa cace yang'anirani, ndi kudziwa ngaka zonse alikubisalamo iye, nimubwere kwa ine ndi mau otsimikizika, pomwepo ndidzamuka nanu; ndipo akakhala m'dzikomo, ndidzampwaira pakati pa mabanja onse a Yuda.
24 Ndipo iwo ananyamuka, namuka ku Zifi asanapiteko Sauli; koma Davide ndi anthu ace anali ku cipululu ca Maoni, m'cigwa ca kumwera kwa cipululu.
25 Ndipo Sauli ndi anthu ace anamuka kukamfuna. Koma wina anauza Davide; cifukwa cace anatsikira kuthanthweko, nakhala m'cipululu ca Maoni. Ndipo pamene Sauli anamva ici, iye anamlondola Davide m'cipululu ca Maoni.
26 Ndipo Sauli anamuka mbali yina ya phiri, Davide ndi anthu ace kutseri kwace; ndipo Davide anafulumira kuthawa, cifukwa ca kuopa Sauli; popeza Sauli ndi anthu ace anazinga Davide ndi anthu ace kwete kuti awagwire.
27 Koma mthenga unafika kwa Sauli ndi kuti, Mufulumire kubwerera; popeza nkhondo yobvumbulukira ya Afilisti yalowa m'dziko.
28 Comweco Sauli anabwerera polondola Davide, nakakomana ndi Afilisti; cifukwa cace anachula dzina lace la malo aja, Thanthwe lolekanitsa.
29 Ndipo Davide anakwera kucokera kumeneko, nakhalam'ngaka za Engedi.
1 Ndipo kunali, pakubwerera Sauli potsata Afilisti, anamuuza, kuti, Taonani, Davide ali ku cipululu ca Engedi.
2 Tsono Sauli anatenga anthu zikwi zitatu osankhika pakati pa Aisrayeli onse, namuka kukafuna Davide ndi anthu ace m'matanthwe a zinkhoma.
3 Ndipo panjira anafika ku makola a nkhosa, kumene kunali phanga; ndipo Sauli analowa kuti akapfunde mapazi ace. Ndipo Davide ndi anyamata ace analikukhala m'kati mwa phangamo,
4 Ndipo anyamata a Davide ananena naye, Onani, lero ndilo tsiku limene Yehova anati kwa inu, Onani, Ine ndidzapereka mdani wako m'dzanja lako, kuti ukamcitira iye cokukomera. Ndipo Davide ananyamuka, nadula mkawo wa mwinjiro wa Sauli mobisika.
5 Ndipo kunali m'tsogolo mwace kuti a mtima wa Davide unamtsutsa cifukwa adadula mkawo wa mwinjiro wa Sauli.
6 Nati kwa anyamata ace, Mulungu andiletse kucitira ici mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova, kumsamulira dzanja langa, popeza iye ndiye wodzozedwa wa Yehova.
7 Comweco Davide analetsa anyamata ace ndi mau awa, osawaloleza kuukira Sauli. Ndipo Sauli ananyamuka, naturuka m'phangamo, namuka njira yace.
8 Bwino lace Davide yemwe ananyamuka, naturuka m'phangamo, napfuulira Sauli, nati, Mbuye wanga, mfumu. Ndipo pakuceuka Sauli, Davide anaweramira nkhope yace pansi, namgwadira.
9 Davide nanena ndi Sauli, Bwanji mulikusamalira mau a anthu akuti, Onani, Davide afuna kukucitirani coipa.
10 Onani, lero lomwe maso anu anapenya kuti Yehova anakuperekani inu lero m'dzanja langa m'phangamo, ndipo ena anandiuza ndikupheni; koma ndinakulekani, ndi kuti, Sindidzatukulira mbuye wanga dzanja langa; cifukwa iye ndiye wodzozedwa wa Yehova.
11 Ndiponso atate wanga, penyani, inde penyani mkawo wa mwinjiro wanu m'dzanja langa; popeza ndinadula mkawo wa mwinjiro wanu, osakuphani, mudziwe, nimuone kuti mulibe coipa kapena kulakwa m'dzanja langa, ndipo sindinakucimwirani, cinkana inu musaka moyo wanga kuti muugwire,
12 Yehova aweruze pakati pa ine ndi inu; ndipo Yehova adzandibwezera cilango kwa inu; koma dzanja langa silidzakhala pa inu.
13 Monga umanena mwambi wa makolo, kuti, Ucimo uturukira mwa ocimwa; koma dzanja langa silidzakhala pa inu.
14 Nanga mfumu ya Israyeli inaturukira yani; inu mulikupitikitsa yani? Garu wakufa, kapena nsabwe.
15 Cifukwa cace Yehova akhale woweruza, naweruze pakati pa ine ndi inu, nayang'anire, oandigwirire moyo, oandipulumutse m'dzanja lanu.
16 Ndipo kunali, pakutsiriza Davide kulankhula mau awa kwa Sauli, Sauli anati, Ndiwo mau ako kodi, mwana wanga Davide? Sauli nakweza mau ace, nalira misozi.
17 Nati kwa Davide, Iwe ndiwe wolungama woposa ine; popeza unandibwezera zabwino, koma ine ndinakubwezera zoipa.
18 Ndipo unatsimikiza lero lino kuti wandicitira zabwino cifukwa sunandipha pamene Yehova anandipereka m'dzanja lako.
19 Pakuti munthu akapeza mdani wace, adzamleka kodi kuti acoke bwino? Cifukwa cace Yehova akubwezere zabwino pa ici unandicitira ine lero lomwe.
20 Ndipo tsono taona ndidziwa kuti udzakhala mfumu ndithu, ndi kuti ufumu wa Israyeli udzakhazikika m'dzanja lako.
21 Cifukwa cace tsono undilumbirire ndi Yehova, kuti sudzatha mbeu yanga nditamuka ine, ndi kuti sudzaononga dzina langa m'nyumba ya atate wanga.
22 Ndipo Davide analumbirira Sauli. Sauli namuka kwao; koma Davide ndi anthu ace anakwera kumka kungaka.
1 Ndipo Samueli anamwalira; ndi Aisrayeli onse anaunjikana pamodzi nalira maliro ace, namuika m'nyumba yace ku Rama. Davide nanyamuka, natsikira ku cipululu ca Parana.
2 Ndipo panali munthu ku Maoni, amene katundu wace anali ku Karimeli; iyeyu anali womveka ndithu, anali nazo nkhosa zikwi zitatu, ndi mbuzi cikwi cimodzi; ndipo analikusenga nkhosa zace ku Karimeli.
3 Tsono dzina la munthuyo ndiye Nabala, ndi dzina la mkazi wace ndiye Abigayeli; ndiye mkazi wa nzeru yabwino, ndi wa nkhope yokongola; koma mwamunayo anali waphunzo ndi woipa macitidwe ace; ndipo iye anali wa banja la Kalebi.
4 Ndipo Davide anamva kucipululu kuti Nabala alinkusenga nkhosa zace.
5 Davide natuma anyamata khumi, nanena kwa anyamatawo, Mukwere ku Karimeli, mumuke kwa Nabala ndi kundilankhulira iye;
6 ndipo muzitero kwa wodalayo, Mtendere ukhale pa inu, mtendere ukhalenso pa nyumba yanu, ndi mtendere ukhale pa zonse muli nazo.
7 Ndipo tsono ndamva kuti muli nao osenga nkhosa; abusa anu amene anali ndi ife, sitinawacititsa manyazi, ndipo panalibe kanthu kao kadasowa, nthawi yonse anakhala iwo ku Karimeli.
8 Mufunse anyamata anu, adzakuuzani; cifukwa cace muwakomere mtima anyamata awa, pakuti tirikufika tsiku labwino; mupatse ciri conse muli naco m'dzanja lanu, kwa anyamata anu, ndi kwa mwana wanu Davide.
9 Ndipo pakufika anyamata a Davide, analankhula ndi Nabala monga mau aja onse m'dzina la Davide, naleka.
10 Koma Nabala anayankha anyamata a Davide nati, Davide ndani? ndi mwana walese ndani? Makono ano pali anyamata ambiri akungotaya ambuye ao.
11 Kodi ndidzatenga mkate wanga, ndi madzi anga, ndi nyama imene ndinaphera osenga nkhosa anga, ndi kuzipatsa anthu amene sindidziwa kumene afumira?
12 Comweco anyamata a Davide anatembenukira ku njira yao, nabwerera, nadza namuuza monga mwa mau onse awa.
13 Ndipo Davide anati kwa anthu ace, Munthu yense wa inu amangirire lupanga lace. Namangirira munthu yense lupanga lace; ndi Davide yemwe anamangirira lupanga lace; ndipo anakwera kumtsata Davide monga anthu mazana anai, koma mazana awiri anadika akatundu.
14 Koma mnyamata wina anauza Abigayeli, mkazi wa Nabala, kuti, Onani, Davide anatumiza mithenga akucokera kucipululu kulankhula mbuye wathu; koma iye anawakalipira.
15 Koma anthu aja anaticitira zabwino ndithu, sanaticititsa manyazi, ndi panalibe kanthu kadatisowa, nthawi zonse tinali kuyenderana nao kubusa kuja;
16 iwo anatikhalira ngati linga usana ndi usiku, nthawi yonse tinali nao ndi kusunga nkhosazo.
17 Cifukwa cace tsono mudziwe ndi kulingalira cimene mudzacita; popeza anatsimikiza mtima kucitira coipa mbuye wathu, ndi nyumba yace yonse; popeza iye ali woipa, ndipo munthu sakhoza kulankhula naye.
18 Pomwepo Abigayeli anafulumira, natenga mikate mazana awiri, ndi zikopa ziwiri za vinyo, nkhosa zisanu zoocaoca, ndi miyeso isanu ya tirigu wokazinga, ndi ncinci za mphesa zouma zana limodzi, ndi ncinci za nkhuyu mazana awiri, naziika pa aburu.
19 Nati kwa anyamataace, Nditsogolereni; onani ndidza m'mbuvo mwanu. Koma sanauza mwamuna wace Nabala.
20 Ndipo kudatero pakuberekeka iye pa buru wace, natsikira pa malo obisika a m'phirilo, onani, Davide ndi anthu ace analikutsikira kwa iye; iye nakomana nao.
21 Koma Davide adanena, Zoonadi ndasunga cabe zace zonse za kaja kanali nazo m'cipululu, sikadasowa kanthu ka zace zonse; ndipo iye anandibwezera zoipa m'malo mwa zabwino.
22 Mulungu alange adani a Davide, ndi kuonjezerapo, ngati ndisiyapo kufikira kuunika kwa m'mawa, kanthu konse ka iye, kangakhale kamwana kamphongo.
23 Ndipo Abigayeli pakuona Davide, anafulumira kutsika pa bum, nagwa pamaso pa Davide nkhope yace pansi, namgwadira,
24 Ndipo atagwadira pa mapazi ace anati, Pa ine, mbuye wanga, pa ine pakhale ucimowo; ndipo mulole mdzakazi wanu alankhule m'makutu anu, nimumvere mau a mdzakazi wanu.
25 Mbuye wanga, musasamalire munthu uyu woipa, ndiye Nabala; cifukwa monga dzina lace momwemo iye; dzina lace ndiye Nabala, ndipo ali nako kupusa; koma ine mdzakazi wanu sindinaona anyamata a mbuye wanga, amene munawatumiza.
26 Cifukwa cace tsono, mbuye wanga, pali Yehova, ndipo pali moyo wanu, popeza Yehova anakuletsani kuti mungakhetse mwazi, ndi kudzibwezera cilango ndi dzanja la inu nokha, cifukwa cace adani anu, ndi iwo akufuna kucitira mbuye wanga coipa, akhale ngati Nabala.
27 Ndipo mphatso iyi mdzakazi wanu ndatengera mbuye wanga, ipatsidwe kwa anyamata akutsata mbuye wanga.
28 Mukhululukire kulakwa kwa mdzakazi wanu; pakuti Yehova adzapatsadi mbuye wanga banja lokhazikika, pakuti mbuyanga amaponya nkhondo za Yehova; ndipo mwa inu simudzapezeka coipa masiku anu onse.
29 Ngakhale anauka anthu kukulondolani, ndi kufuna moyo wanu, koma moyo wa mbuye wanga udzamangika m'phukusi la amoyo lakukhala ndi Yehova Mulungu wanu; koma iye adzaponya miyoyo ya adani anu kuwataya monga coturuka m'coponyera mwala.
30 Ndipo kudzali, pamene Yehova anacitira mbuye wanga monga mwa zabwino zonse adalankhula za inu, ndipo adadzaika inu mukhale kalonga wa Israyeli;
31 mudzakhala opanda cakudodoma naco, kapena cakusauka naco mtima wa mbuye wanga, cakuti munakhetsa mwazi wopanda cifukwa, kapena kuti mbuye wanga anabwezera cilango; ndipo Yehova akadzacitira mbuye wanga zabwino, pamenepo mukumbukile mdzakazi wanu.
32 Ndipa Davide anati kwa Abigayeli, Alemekezedwe Yehova Mulungu wa Israyeli, amene anakutumiza lero kudzandicingamira ine;
33 ndipo, kudalitsike kucenjera kwako, nudalitsike iwe, pakuti unandiletsa kusakhetsa mwazi, ndi kusabwezera cilango ndi dzanja la ine ndekha.
34 Pakuti ndithu, Pali Yehova Mulungu wa Israyeli, amene anandiletsa lero kusapweteka iwe, ukadapanda kufulumira kubwera kundicingamira, zoonadi sindikadasiyira Nabala kufikira kutaca kanthu konse, ngakhale mwana wamwamunammodzi.
35 Comweco Davide analandira m'dzanja lace zimene iye anamtengera; nanena naye, Ukwere kwanu mumtendere; ona, ndamvera mau ako, ndabvomereza nkhope yako.
36 Ndipo Abigayeli anafika kwa Nabala; ndipo, onani, anali ndi madyerero m'nyumba mwace, monga madyerero a mfumu; ndi mtima wa Nabala unasekera kwambiri m'kati mwace, pakuti analedzera kwambiri; m'mwemo uyo sadamuuza kanthu konse, kufikira kutaca.
37 Tsono m'mawa vinyo atamcokera Nabala, mkazi wace anamuuza zimenezi; ndipo mtima wace unamyuka m'kati mwace, iye nasanduka ngati mwala.
38 Ndipo kunali, atapita masiku khumi, Yehova anamkantha Nabala, nafa.
39 Ndipo pamene Davide anamva kuti Nabala adamwalira, iye anati, Alemekezedwe Yehova, amene anaweruza mrandu wa mtonzo wanga wocokera ku dzanja la Nabala, naletsa mnyamata wace pa coipa; ndipo Yehova anabwezera pamutu pa Nabala coipa cace. Ndipo Davide anatumiza wokamfunsira Abigayeli, zakuti amtengere akhale mkazi wace.
40 Ndipo anyamata a Davide pakufika kwa Abigayeli ku Karimeli, analankhula naye, nati, Davide anatitumiza kwa inu, kukutengani, mukhale mkazi wace.
41 Ndipo iye ananyamuka, nawerama nkhope yace pansi, nati, Onani, mdzakazi wanu ali kapolo wakusambitsa mapazi a anyamata a mbuye wanga.
42 Ndipo Abigayeli anafulumira nanyamuka, nakwera pa bum, pamodzi ndi anamwali ace asanu akumtsata; natsatira mithenga ya Davide, nakhala mkazi wace.
43 Davide anatenganso Ahinoamu wa ku Yezreeli, ndipo onse awiri anakhala akazi ace.
44 Pakuti Sauli anapatsa Mikala, mwana wace, mkazi wa Davide, kwa Paliti mwana wa Loisi, wa ku Galimu.
1 Ndipo Azifi anafika kwa Sauli ku Gibeya, nati, Kodi Davide sali kubisala m'phiri la Hagila, kupenya kucipululu!
2 Ndipo Sauli ananyamuka, natsikira ku cipululu ca Zifi, ndi anthu zikwi zitatu a Israyeli osankhika, kukafuna Davide m'cipululu ca Zifi.
3 Sauli namanga zithando m'phiri la Hagila kupenya kucipululu kunjira, Koma Davide anakhala kucipululu, naona kuti Sauli alikumfuna kucipululu komweko.
4 Cifukwa cace Davide anatumiza ozonda, nazindikira kuti Sauli anabwera ndithu,
5 Ndipo Davide ananyamuka nafika pamalo pala Sauli anamangapo; ndipo Davide adaona pogona Sauli, ndi Abineri mwana wa Neri kazembe wa khamu lace; ndipo Sauli anagona pakati pa linga la magareta, ndipo anthu adamanga zithando pomzinga pace.
6 Pamenepo Davide anayankha nati kwa Ahimeleki Mhiti, ndi Abisai mwana wa Zeruya, mbale wace wa Yoabu, nati, Adzatsikira nane ndani kumisasako kwa Sauli? Nati Abisai, Nditsika nanu ndine.
7 Comweco Davide ndi Abisai anafika kwa anthuwo usiku; ndipo onani, Sauli anagona tulo m'kati mwa linga la magareta, ndi mkondo wace wozika kumutu kwace; ndi Abineri ndi anthuwo anagona pomzinga iye.
8 Ndipo Abisai anati kwa Davide, Lero Mulungu wapereka mdani wanu m'dzanja lanu; ndiloleni ndimpyoze ndi mkondo, kamodzi kokha, sindidzampyoza kawiri.
9 Koma Davide ananena ndi Abisai, Usamuononge, ndani adzasamula dzanja lace pa wodzozedwa wa Mulungu, ndi kukhala wosacimwa?
10 Nati Davide, Pali Yehova, Yehova adzamkantha iye; kapena tsiku la imfa yace lidzafika; kapena adzatsikira kunkhondo, nadzafako.
11 Yehova andiletse ine kusamula dzanja langa pa wodzozedwa wa Yehova; koma utenge mkondowo uli kumutu kwace, ndi cikho ca madzi, ndipo tiyeni, timuke.
12 Comweco Davide anatenga mkondowo, ndi cikho ca madzi ku mutu wa Sauli nacoka iwowa, osawaona munthu, kapena kuzidziwa, kapena kugalamuka; pakuti onse anati m'tulo; popeza tulo tatikuru tocokera kwa Yehova tinawagwira onse.
13 Ndipo Davide anaolokera kutsidya, naima patali pamwamba pa phiri; pakati pao panati danga lalikuru;
14 ndipo Davide anaitana anthuwo, ndi Abineri mwana wa Neri, nati, Suyankha kodi Abineri? Tsono Abineri anayankha, nati, Ndiwe yani amene uitana mfumuyo?
15 Davide nati kwa Abineri, Si ndiwe mwamuna weni weni kodi? ndani mwa Aisrayeli afanafana ndi iwe? Unalekeranji tsono kudikira mbuye wako, mfumuyo? pakuti anafika wina kudzaononga mfumu, mbuye wako.
16 Ici unacicita siciri cabwino. Pali Yehova, muyenera kufa inu, cifukwa simunadikira mbuye wanu, wodzozedwa wa Yehova. Ndipo tsono, penyani mkondo wa mfumu ndi cikho ca madzi zinali kumutu kwace ziri kuti?
17 Ndipo Sauli anazindikira mau ace a Davide, nati, Ndi mau ako awa, mwana wanga Davide? Nati Davide, Ndi mau anga mfumu, mbuye wanga.
18 Nati iye, Cifukwa ninji mbuye wanga amalondola mnyamata wace? pakuti ndacitanji? kapena m'dzanja langa muli coipa cotani?
19 Cifukwa cace mbuye wanga mfumu amvere mau a kapolo wace. Ngati ndi Yehova anakuutsirani inu kutsutsana ndi ine, alandire copereka; koma ngati ndi ana a anthu, atembereredwe pamaso pa Yehova, pakuti anandipitikitsa lero kuti ndisalandireko colowa ca Yehova, ndi kuti, Muka, utumikire milungu yina.
20 Cifukwa cace tsono, mwazi wanga usagwe pansi kutati ndi Yehova; pakuti mfumu ya Israyeli yaturuka kudzafuna nsabwe, monga munthu wosaka nkhwali pamapiri.
21 Pamenepo Sauli anati, Ndinacimwa; bwera, mwana wanga Davide; pakuti sindidzakucitiranso coipa, popeza moyo wanga unati wa mtengo wapatali pamaso pako lero; ona, ndinapusa ndi kulakwa kwakukuru.
22 Davide nayankha, nati, Tapenyani lmkondo wa mfumu Abwere mnyamata wina kuutenga.
23 Ndipo Yehova adzabwezera munthu yense cilungamo cace ndi cikhulupiriko cace, popeza Yehova anakuperekani lero m'dzanja langa, koma sindinalola kutukulira dzanja langa pa wodzozedwa wa Yehova,
24 Ndipo onani, monga lero ndinasamalira ndithu moyo wanu, momwemo usamaliridwe ndithu moyo wanga pamaso pa Yehova, ndipo iye andipulumutse ku masautso onse.
25 Pomwepo Sauli anati kwa Davide, Udalitsike iwe, mwana wanga Davide; udzacita ndithu camphamvu, nudzapambana. Comweco Davide anamuka, ndipo Sauli anabwera kwao.
1 Ndipo Davide ananena mumtima mwace, Tsiku tina Sauli adzandipha; palibe cina condikomera koma kuti ndithawire ku dziko la Afilisti; ndipo Sauli adzakhala kakasi cifukwa ca ine, osandifunanso m'malire onse a Israyeli, momwemo ndidzapulumuka m'dzanja lace.
2 Ndipo Davide ananyamuka, naoloka pamodzi ndi anthu mazana asanu ndi limodzi amene anali naye, nafika kwa Akisi mwana wa Maoki, mfumu ya ku Gati.
3 Ndipo Davide anakhala ndi Akisi ku Gati, iye ndi anthu ace, munthu yense ndi a pabanja pace, inde Davide ndi akazi ace awiri, Ahinoamu wa ku Jezreeli, ndi Abigayeli wa ku Karimeli, mkazi wa Nabala.
4 Ndipo anauza Sauli kuti Davide anathawira ku Gati; ndipo iye sanamfunanso.
5 Ndipo Davide anati kwa Akisi, Ngati mwandikomera mtima, andipatse malo kumudzi kwina kumiraga, kuti ndikakhale kumeneko; pakuti mnyamata wanu adzakhala bwanji m'mudzi wacifumu pamodzi ndi inu?
6 Ndipo Akisi anampatsa Zikilaga tsiku lomweli; cifukwa cace Zikilaga ndi wa mafumu a Yuda kufikira lero lomwe.
7 Ndipo kuwerenga kwace kwa masiku Davide anakhala ku dziko la Afilisti ndiko caka cimodzi ndi miyezi inai.
8 Ndipo Davide ndi anthu ace anakwera, nathira nkhondo yobvumbulukira pa Agesuri, ndi Agirezi, ndi Aamaleki; pakuti awa ndiwo anthu akale a m'dziko lija, njira ya ku Suri kufikira ku dziko la Aigupto.
9 Ndipo Davide anapasula dzikolo, sanasunga ndi moyo mwamuna kapena wamkazi; natenga nkhosa, ndi ng'ombe, ndi aburu, ndi ngamila, ndi zobvala; nabwera nafika kwa Akisi.
10 Ndipo Akisi anati, Wapooyana nkhondo ndi yani lero? Nati Davide, Ndi a kumwera kwa Ayuda, ndi a kumwera kwa Ayerameli, ndi a kumwera kwa Akeni.
11 Ndipo Davide sadasunga wamoyo mwamuna kapena mkazi, kubwera nao ku Gati; popeza adati, Kuti angatiulule, ndi kuti, Davide anatero, ndi makhalidwe ace ndi otere, masiku onse akukhala ku dziko la Afilisti.
12 Ndipo Akisi anakhulupirira Davide, nati Anadziipitsa ndithu pakati pa anthu a Israyeli, cifukwa cace iye adzakhala mnyamata wanga cikhalire.
1 Ndipo kunali masiku aja, Afilisti anasonkhanitsa pamodzi makamu ao onse kunkhondo, kuti akaponyane ndi Aisrayeli. Ndipo Akisi ananena ndi Davide, Dziwa kuti zoonadi, udzaturuka nane ndi nkhondo, iwe ndi anthu ako.
2 Ndipo Davide anati kwa Akisi, Potero mudzadziwe cimene mnyamata wanu adzacita. Ndipo Akisi anati kwa Davide, Cifukwa cace ndidzakuika iwe ukhale wondisungira moyo wanga masiku onse.
3 M'menemo Samueli ndipo atafa, ndipo Aisrayeli onse atalira maliro ace, namuika m'Rama, m'mudzi mwao. Ndipo Sauli anacotsa m'dzikomo obwebweta onse, ndi aula onse.
4 Ndipo Afilisti anasonkhana, nadza namanga misasa ku Sunemu; ndipo Sauli anasonkhanitsa Aisrayeli onse, namanga iwo ku Giliboa.
5 Ndipo pamene Sauli anaona khamu la Afilisti, anaopa, ndi mtima wace unanjenjemera kwakukuru.
6 Ndipo pamene Sauli anafunsira kwa Yehova, Yehova sanamyankha ngakhale ndi maloto, kapena ndi Urimu, kapena ndi aneneri.
7 Tsono Sauli anati kwa anyamata ace, Mundifunire mkazi wobwebweta, kuti ndimuke kwa iye ndi kumfunsira. Ndipo anyamata ace anati kwa iye, Onani ku Endori kuli mkazi wobwebweta.
8 Ndipo Sauli anadzizimbaitsa nabvala zobvala zina, nanka iye pamodzi ndi anthu ena awiri, nafika kwa mkaziyo usiku; nati iye, Undilotere ndi mzimu wobwebwetawo, nundiukitsire ali yense ndidzakuchulira dzina lace.
9 Ndipo mkaziyo ananena naye, Onani, mudziwa cimene anacita Sauli, kuti analikha m'dzikomo obwebweta onse, ndi aula; cifukwa ninji tsono mulikuchera moyo wanga msampha, kundifetsa.
10 Ndipo Sauli anamlumbirira kwa Yehova, nati, Pali Yehova, palibe cilango cidzakugwera cifukwa ca cinthu ici.
11 Pomwepo mkaziyo anati, Ndikuukitsireni yani? Nati iye, Undiukitsire Samueli.
12 Ndipo mkaziyo pakuona Samueli, anapfuula ndi mau akuru; ndi mkaziyo analankhula ndi Sauli, nati, Munandinyengeranji? popeza inu ndinu Sauli.
13 Ndipo mfumuvo inanena naye, Usaope, kodi ulikuona ciani? Mkaziyo nanena ndi Sauli, Ndirikuona milungu irikukwera kuturuka m'kati mwa dziko.
14 Ndipo ananena naye, Makhalidwe ace ndi otani? nati iye, Nkhalamba irikukwera yobvala mwinjiro. Pamenepo Sauli anazindikira kuti ndi Samueli, naweramitsa nkhope yace pansi, namgwadira.
15 Ndipo Samueli ananena ndi Sauli, Wandibvutiranji kundikweretsa kuno? Sauli nayankha, Ndirikusautsika kwambiri, pakuti Afilisti aponyana nkhondo ndi ine, ndipo Mulungu anandicokera, osandiyankhanso, kapena ndi aneneri, kapena ndi maloto; cifukwa cace ndakuitanani, kuti mundidziwitse cimene ndiyenera kucita.
16 Ndip'o Samueli ananena naye, Ndipo undifunsiranji ine, popeza Yehova anakucokera, nasandulika mdani wako?
17 Ndipo Yehova yekha wacita monga ananena pakamwa panga; ndipo Yehova wang'amba ufumuwo, kuucotsa m'dzanja lako, ndi kuupatsa mnansi wako, ndiye Davide.
18 Cifukwa sunamvera mau a Yehova, ndi kukwaniritsa mkwiyo wace woopsa pa Ameleki, cifukwa cace Yehova wakucitira cinthu ici lero.
19 Ndiponso Yehova adzapereka Israyeli pamodzi ndi iwe m'dzanja la Afilisti; ndipo mawa iwe ndi ana ako mudzakhala kuli ine; Yehova adzaperekanso khamu la Aisrayeli m'dzanja la Afilisti.
20 Pomwepo Sauli anagwa pansi tantha, naopa kwakukuru, cifukwa ca mau a Samueli; ndipo analibe mphamvu; pakuti tsiku lonse ndi usiku wace wonse anakhala osadya kanthu.
21 Ndipo mkaziyo anafika kwa Sauli, naona kuti ali wobvutika kwambiri, nanena naye, Onani, mdzakazi wanu anamvera mau anu, ndipo ndinataya moyo wanga, ndi kumvera mau anu munalankhula ndi ine.
22 Cifukwa cace tsono, mumverenso mau a mdzakazi wanu, nimundilole kuika kakudya pamaso panu; ndipo mudye, kuti mukhale ndi mphamvu pakumuka.
23 Koma iye anakana, nati, Sindifuna kudya. Koma anyamata ace, pamodzi ndi mkaziyo anamkangamiza; iyenamvera mau ao. Comweco anauka pansi, nakhala pakama.
24 Ndipo mkaziyo anali ndi mwana wa ng'ombe wonenepa m'nyumbamo; ndipo anafulumira, namupha, natenga ufa naukanyanga mkate wopanda cotupitsa;
25 nabwera nazo kwa Sauli ndi kwa anyamata ace; nadya iwowa. Atatero ananyamuka, nacoka usiku womwewo.
1 Tsono Afilisti anasonkhanitsa makamu ao onse ku Afeki; ndipo Aisrayeli anamanga ku citsime ca m'Jezreeli.
2 Ndipo akalonga a Afilisti ananyamuka ndi mazana ao ndi zikwi zao; ndipo Davide ndi anthu ace ananyamuka ndi a pambuyo pamodzi ndi Akisi.
3 Ndipo akalonga a Afilisti anati, Ahebri awa acitanji pano? Ndipo Akisi ananena kwa akalonga a Afilisti, Uyu si Davide uja mnyamata wa Sauli, mfumu ya Israyeli, amene wakhala nane masiku awa kapena zaka izi, ndipo sindinapeza kulakwa mwa iye, kuyambira tsiku lija anaphatikana nane kufikira lero.
4 Koma akalonga a Afilisti anapsa naye mtima; nanena naye akalonga a Afilisti, Bwezani munthuyu, abwerere kumalo kwace kumene munamuikako, asatsikire nafe kunkhondo, kuti kunkhondoko angasanduke mdani wathu; pakuti uyu adzadziyanjanitsa ninji ndi mfumu yace? Si ndi mitu ya anthu awa?
5 Uyu si Davide kodi amene anamthirirana mang'ombe m'magulu ao, kuti, Sauli anapha zikwi zace, Koma Davide zikwi zace zankhani?
6 Ndipo Akisi anaitana Davide, nanena naye, Pali Yehova, wakhala woongoka mtima, ndipo kuturuka kwako ndi kubwera kwako pamodzi ndi ine m'gulumo kundikomera; pakuti sindinaona coipa mwa iwe kuyambira tsiku la kufika kwako kufikira lero; koma akalongawo sakukomera mtima.
7 Cifukwa cace, bwerera, numuke mumtendere, kuti angaipidwe mtima nawe akalonga a Afilisti.
8 Ndipo Davide ananena ndi Akisi, Koma ndinacitanji? Ndipo munapeza ciani mu mnyamata wanu nthawi yonse ndiri pamaso panu kufikira lero, kuti sindingapite kukaponyana nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?
9 Ndipo Akisi anayankha nanena ndi Davide, Ndidziwa kuti pamaso panga uli wabwino, ngati mthenga wa Mulungu; koma akalonga a Afilisti anena, iye asamuke nafe kunkhondoko.
10 Cifukwa cace ulawirire m'mawa pamodzi ndi anyamata a mbuye wako amene anabwera nawe; ndipo mutauka m'mawa, mumuke kutaca.
11 Comweco Davide analawirira, iye ndi anthu ace, kuti amuke m'mawa ndi kubwera ku dziko la Afilisti. Ndipo Afilisti anakwera ku Jezreeli.
1 Ndipo kunali, pakufika Davide ndi anthu ace ku Zikilaga tsiku lacitatu, Aamaleki adaponya nkhondo yobvumbulukira kumwera, ndi ku Zikilaga, nathyola Zikilaga nautentha ndi moto;
2 nagwira akazi ndi onse anali m'mwemo, akuru ndi ang'ono; sanapha mmodzi, koma anawatenga, namuka.
3 Ndipo pamene Davide ndi anthu ace anafika kumudziko, onani, unatenthedwa ndi moto; ndi akazi ao ndi ana ao amuna ndi akazi anatengedwa ukapolo.
4 Ndipo Davide ndi anthu amene anali naye anakweza mau ao, nalira misozi, kufikira analibe mphamvu yakuliranso.
5 Ndipo akazi awiri a Davide anatengedwa ukapolo, Ahinoamu wa ku Jezreeli ndi Abigayeli mkazi wa Nabala wa ku Karimeli.
6 Ndipo Davide anadololoka kwambiri, pakuti anthu ananena za kumponya iye miyala, pakuti mtima wao wa anthu onse unali ndi cisoni, yense cifukwa ca ana ace amuna ndi akazi. Koma Davide anadzilimbikitsa mwa Yehova Mulungu wace.
7 Ndipo Davide ananena ndi Abyatara wansembeyo, mwana wa Ahimeleki, Unditengere kuno efodi. Abyatara nabwera ndi efodi kwa Davide.
8 Ndipo Davide anafunsira kwa Yehova, nati, Ndikalondola khamulo ndidzalipeza kodi? Ndipo anamyankha kuti, Lonriola, pakuti zoonadi udzawapeza, ndi kulanditsa zonse.
9 Comweco Davide anamuka, iye ndi anthu mazana asanu ndi limodzi anali naye, nafika kukamtsinje Besori, pamenepo anatsala ena.
10 Ndipo Davide anawalondola, iye ndi anthu mazana anai; koma anthu mazana awiri anatsala m'mbuyo, cifukwa analema, osakhoza kuoloka kamtsinje Besori.
11 Ndipo ena anapeza M-aigupto kuthengo, nabwera naye kwa Davide, nampatsa cakudya, nadya iye; nampatsanso madzi kumwa;
12 nampatsanso cigamphu ca ncinci ya nkhuyu ndi ncinci ziwiri za mphesa; ndipo atadya, moyo wace unabweranso mwa iye; pakuti adagona masiku atatu ndi usiku wao, osadya cakudya, osamwa madzi.
13 Pamenepo Davide ananena naye, Ndiwe wa yani? ufumira kuti? Nati iye, Ndiri mnyamata wa ku Aigupto, kapolo wa M-amaleki; mbuye wanga anandisiya, cifukwa ndinayambodwala apita masiku atatu.
14 Tinathira nkhondo kumwera kwa Akereti ndi ku dziko lija la Ayuda, ndi kumwera kwa Kalebi; ndipo tinatentha mudzi wa Zikilaga ndi moto.
15 Ndipo Davide ananena naye, Kodi udzanditsogolera kufikira ku khamulo? Nati iye, Mundilumbirire kwa Mulungu, kuti simudzandipha, kapena kundipereka m'dzanja la mbuye wanga, ndipo ndidzatsika nanu kuli khamu limene.
16 Ndipo pamene anatsika naye, onani, iwo anabalalika apo ponse, analinkudya, ndi kumwa, ndi kudyerera, cifukwa ca cofunkha zambiri anazitenga ku dziko la Afilisti, ndi ku dziko la Yuda.
17 Ndipo Davide anawakantha kuyambira madzulo kufikira usiku wa mawa wace; ndipo panalibe munthu mmodzi wa iwowa anapulumuka, koma anyamata mazana anai oberekeka pa ngamila, nathawa.
18 Ndipo Davide analanditsa zonse anazitenga Aamaleki, napulumutsa akazi ace awiri.
19 Ndipo sikanasoweka kanthu, kakang'ono kapena kakakuru, ana amuna kapena ana akazi, kapena cuma kapena dna ciri conse ca zija anazitenga iwowa; Davide anabwera nazo zonse.
20 Ndipo Davide anatenga nkhosa zonse ndi ng'ombe zonse, zimene anazipitikitsa patsogolo pa zoweta zao zao, nati, Izi ndi zofunkha za Davide.
21 Ndipo Davide anafika kuli anthu mazana awiri amene analema osakhoza kutsata Davide, amenenso anawakhalitsa kukamtsinje Besori; ndipo iwowa anaturuka kucingamira Davide, ndi amene anali naye; ndipo pakuyandikira Davide anawafunsa ngati ali bwanji.
22 Pamenepo anthu oipa onse, ndi opanda pace a iwo amene anapita ndi Davide anayankha nati, Popeza sadamuka nafe sitidzawapatsa kanthu ka zofunkha tidazilanditsa, koma kwa munthu yense mkazi wace ndi ana ace, kuti acoke nao namuke.
23 Davide nati, Simudzatero, abale anga inu, ndi zimene anatipatsa ife Yehova, amene anatisunga, napereka m'dzanja lathu khamu lija linadza kumenyana nafe.
24 Ndipo ndani adzabvomerezana nanu mrandu uwu? Pakuti monga gawo lace la iye wakumuka kunkhondoko, momwemo lidzakhala gawo lace la iye wakukhala ndi akatundu, adzagawana cimodzimodzi.
25 Ndipo kuyambira tsiku lija kufikira lero lomwe anaika ici, cikhale lemba ndi ciweruzo pa Aisrayeli.
26 Ndipo pamene Davide anafika ku Zikilaga, anatumizako za zofunkhazo kwa akuru a Yuda, ndiwo abwenzi ace, nati, Siyi mphatso yanu ya zofunkha za adani a Yehova.
27 Anatumiza kwa iwo a ku Beteli, ndi kwa iwo a ku Ramoti wa kumwela, ndi kwa iwo a ku Yatiri;
28 ndi kwa iwo a ku Aroeri, ndi kwa iwo a ku Sifimoti, ndi kwa iwo a ku Estimoa;
29 ndi kwa iwo a ku Rakala, ndi kwa iwo a m'midzi ya Ayerameli, ndi kwa iwo a m'midzi ya Akeni;
30 ndi kwa iwo a ku Horima, ndi kwa iwo a ku Korasani, ndi kwa iwo a ku Ataki;
31 ndi kwa iwo a ku Hebroni, ndi kumalo konse kumene Davide ndi anthu ace adafoyendayenda.
1 Ndipo Afilisti anaponyana ndi Aisrayeli; Aisrayeli nathawa pamaso pa Afilisti, nagwa olasidwa m'phiri la Giliboa.
2 Ndipo Afilisti anapitikitsa, osawaleka Sauli ndi ana ace; ndipo Afilisti anapha Jonatani, ndi Abinadabu, ndi Malikisua, ana a Sauli.
3 Ndipo nkhondoyo inamkulira Sauli kwambiri, oponya mibvi nampeza; ndipo iye anasautsika kwakukuru cifukwa ca oponya mibviyo.
4 Tsono Sauli ananena ndi wonyamula zida zace, Solola lupanga lako, undipyoze nalo; kuti osadulidwa awa angabwere ndi kundipyoza, ndi kundiseka, Koma woo nyamula zida zace anakana; cifukwa anaopa ndithu. Cifukwa cace Sauli anatenga lupanga lace naligwera.
5 Ndipo pakuona kuti Sauli anafa, wonyamula zida zace yemwe, anagwera lupanga lace, nafera limodzi ndi iye.
6 Comweco adamwalira pamodzi Sauli ndi ana ace atatu, ndi wonyamula zida zace, ndi anthu ace onse, tsiku lomwe lija.
7 Ndipo pamene Aisrayeli akukhala tsidya lina la cigwa, ndi iwo akukhala tsidya la Yordano, anaona kuti Aisrayeli alikuthawa, ndi kuti Sauli ndi ana ace anafa, iwowa anasiya midzi yao, nathawa; ndipo Afilisti anadza nakhala m'menemo.
8 Ndipo kunali m'mawa mwace, pakubwera Afilisti kubvula akufawo, anapeza Sauli ndi ana ace atatu ali akufa m'phiri la Giliboa.
9 Ndipo anadula mutu wace, natenga zida zace, natumiza m'dziko lonse la Afilisti mithenga yolalikira ku nyumba ya milungu yao, ndi kwa anthu.
10 Ndipo anaika zida zace m'nyumba ya Asitarote; napacika mtembo wace ku linga la ku Betisani.
11 Koma pamene a ku Jabezi Gileadi anamva zimene Afilisti anamcitira Sauli,
12 ngwazi zonse zinanyamuka ndi kucezera usiku kuyenda, natenga mtembo wa Sauli, ndi mitembo ya ana ace, pa linga la Betisani; nafika ku Jabezi Gileadi naitentha kumeneko.
13 Natenga mafupa ao nawaika patsinde pa mtengo uli m'Jabezi, nasala kudya masiku asanu ndi awiri.