1

1 PAULO, mtumwi (wosacokera kwa anthu, kapena mwa munthu, koma mwa Yesu Kristu, ndi Mulungu Atate, amene anamuukitsa iye kwa akufa),

2 ndi abale onse amene ali pamodzi ndi ine, kwa Mipingo ya ku Galatiya:

3 Cisomo kwa inu, ndi mtendere wa kwa Mulungu Atate, ndi Ambuye wathu Yesu Kristu,

4 amene anadzipereka yekha cifukwa ca macimo athu, kuti akatilanditse ife m'nyengo ya pansi pano yino yoipa, monga mwa cifuniro ca Mulungu ndi Atate wathu;

5 yemweyo akhale nao ulemerero ku nthawi za nthawi. Amen.

6 Ndizizwa kuti msanga motere mulikutunsika kwa iye amene anakuitanani m'cisomo ca Kristu, kutsata uthenga wabwino wina;

7 umene suli wina; koma pali ena akubvuta inu, nafuna kuipsa Uthenga Wabwino wa Kristu.

8 Koma ngakhale ife, kapena mngelo wocokera Kumwamba, ngati akakulalikireni uthenga wabwino wosati umene tidakulalikirani ife, akhale wotembereredwa.

9 Monga tinanena kale, ndipo ndinenanso tsopano apa, ngati wina akulalikirani uthenga wabwino wosati umene mudaulandira, akhale wotembereredwa.

10 Pakuti kodi ndikopa anthu tsopano, kapena Mulungu? Kapena kodi ndifuna kukondweretsa anthu? Ndikadakhala wokondweretsabe anthu, sindikadakhala kapolo wa Kristu.

11 Pakuti ndikudziwitsani inu, abale, za Uthenga Wabwinowo wolalikidwa ndi ine, kuti suli monga mwa anthu.

12 Pakutitu sindinaulandira kwa munthu, kapena sindinauphunzira, komatu unadza mwa bvumbulutso la Yesu Kristu.

13 Pakuti mudamva za makhalidwe anga kale mwa Ciyuda, kuti ndinalondalonda Mpingo wa Mulungu koposa, ndi kuupasula,

14 ndipo ndinawaposa ndi kutsogola mwa Ciyuda ambiri a msinkhu wanga mwa mtundu wanga, ndipo ndinakhala wacangu koposa pa miyambo ya makolo anga.

15 Koma pamene padakondweretsa Mulungu, amene anandipatula, ndisanabadwe, nandiitana ine mwa cisomo cace,

16 kuti abvumbulutse Mwana wace mwa ine, kuti ndimlalikire iye mwa amitundu; pomwepo sindinafunsana ndi thupi ndi mwazi:

17 kapena kukwera kunka ku Yerusalemu sindinankako kwa iwo amene anakhala atumwi ndisanakhale mtumwi ine, komatu ndinamuka ku Arabiya, ndipo ndinabweranso ku Damasiko.

18 Pamenepo patapita zaka zitatu, ndinakwera kunka ku Yerusalemu kukazindikirana naye Kefa, ndipo ndinakhala kwa iye masiku khumi ndi asanu.

19 Koma wina wa atumwi sindinamuona, koma Yakobo mbale wa Ambuye.

20 Ndipo izi ndikulemberani inu, taonani, pamaso pa Mulungu sindinama ine.

21 Pamenepo ndinadza ku mbali za Suriya ndi Kilikiya.

22 Koma ndinali wosadziwika nkhope yanga kwa Mipingo ya ku Yudeya ya mwa Kristu;

23 koma analinkumva kokha, kuti, iye wakutilondalonda ife kale, tsopane alalikira cikhulupiriroco ada cipasula kale;

24 ndipo analemekeza Mulungu mwaine.

2

1 Pamenepo popita zaka khumi ndi zinai ndinakweranso kunka ku Yerusalemu pamodzi ndi Bamaba, ndinamtenganso Tito andiperekeze.

2 Koma ndinakwera kunkako mobvumbulutsa; ndipo ndinawauza Uthenga Wabwino umene ndiulalikira kwa amitundu; koma m'tseri kwa iwo omveka, kuti kapena ndingathamange, kapena ndikadathamanga cabe.

3 Komatu ngakhale Tito, amene anali ndi ine, ndiye Mhelene, sanamkakamiza adulidwe;

4 ndico cifukwa ca abale onyenga olowezedwa m'tseri, amene analowa m'tseri kudzazonda ufulu wathu umene tiri nao mwa Kristu Yesu, kuti akaticititse iukapolo.

5 Koma sitidawafumukira mowagonjera ngakhale ora limodzi; kuti coonadi ca Uthenga Wabwino cikhalebe ndi inu.

6 Koma iwo akuyesedwa ali kanthu (ngati anali otani kale, kulibe kanthu kwa ine; Mulungu salandira nkhope ya munthu) iwo omvekawo sanandionjezera ine kanthu;

7 koma pena, pakuona kuti anaikiza kwa ine Uthenga Wabwino wa kusadulidwa, monga kwa Petro Uthenga Wabwino wa mdulidwe

8 (pakuti iye wakucita mwa Petro kumtuma kwa odulidwa anacitanso mwa ine kundituma kwa amitundu);

9 ndipo pakuzindikira cisomoco cinapatsidwakwa ine, Yakobo ndi Kefa ndi Yohane, amene anayesedwa mizati, anapatsa ine ndi Bamaba dzanja lamanja la ciyanjano, kuti ife tipite kwa amitundu, ndi iwo kwa mdulidwe;

10 pokhapo kuti tikumbukile aumphawi; ndico comwe ndinafulumira kucicita.

11 Koma pamene Kefa anadza ku Antiokeyandinatsutsana naye pamaso pace, pakuti anatsutsika wolakwa.

12 Pakuti asanafike ena ocokera kwa Yakobo, anadya pamodzi ndi amitundu; koma atadza iwo, anadzibweza, ndi kudzipatula yekha, pakuopa iwo a ku mdulidwe.

13 Ndipo Ayuda otsala anawagwiranso m'maso pamodzi naye; kotero kuti Bamabanso anatengedwa ndi kugwira m'maso kwao.

14 Komatu pamene ndinaona kuti sanalikuyenda koongoka, monga mwa coonadi ca Uthenga Wabwino, ndinati kwa Kefa pamaso pa onse, Ngati inu muli Myuda mutsata makhalidwe a amitundu, ndipo si a Ayuda, mukangamiza bwanji amitundu atsate makhalidwe a Ayuda?

15 Ife ndife Ayuda pacibadwidwe, ndipo sitiri ocimwa a kwaamitundu;

16 koma podziwa kuti munthu sayesedwa wolungama pa: nchito ya lamulo, koma mwa cikhulupiriro ca Yesu Kristu, ifedi tinakhulupirira kwa Yesu Kristu, kuti tikayesedwe olungama ndicikhulupiriro ca Kristu, ndipo si ndi nchito za lamulo; pakuti palibe munthu adzayesedwa wolungama ndi nchito za lamulo.

17 Koma ngati ife, pofuna kuyesedwa olungama mwa Kristu, tipezedwanso tiri ocimwa tokha, kodi Kristu ali mtumikiwa ucimo cifukwa cace? Msatero ai.

18 Pakuti ngati izi zomwezi ndazigumula ndizimanganso, ndidzitsimikizira ndekha ndirt wolakwa.

19 Pakuti ine mwa lamulo ndafa ku lamulo, kuti ndikhale ndi moyo kwa Mulungu.

20 Ndinapacikidwa ndi Kristu; koma ndiri ndi mayo; wosatinso ine ai, koma Kristu ali ndi moyo mwa ine; koma moyo umene ndiri nao: tsopano m'thupi, ndiri nao m'cikhulupiriro ca Mwana wa Mulungu, amene anandikonda, nadzipereka yekha cifukwa ca ine.

21 Sindieiyesa copanda pace cisomo ca Mulungu; pakuti ngati cilungamo ciri mwa Lamulo, Kristu adafa cabe.

3

1 Agalatiya opusa inu, anakulodzani ndani, inu amene Kristu anaonetsedwa pa maso panu, wopacikidwa?

2 ici cokha ndifuna kuphunzira kwa inu, Kodi munalandira Mzimuyo ndi nchito za lamulo, kapena ndi kumva kwa cikhulupiriro?

3 Kodi muli opusa otere? Popeza mudayamba ndi Mzimu, kodi tsopano mutsiriza ndi thupi?

4 Kodi mudamva zowawa zambiri zotere kwacabe? ngatitu kwacabe.

5 Ndipo iye amene akuonjezerani inu Mzimuyo, nacita zimphamvu mwa inu, atero kodi ndi nchito za lamulo, kapena ndi kumva kwa cikhulupiriro?

6 Monga Abrahamu anakhulupirira Mulungu, ndipo kunawerengedwa kwa iye cilungamo,

7 cotero zindikirani kuti iwo a cikhulupiriro ndiwo ana a Abrahamu.

8 Ndipo malembo, pakuoneratu kuti Mulungu adzayesa olungama amitundu ndi cikhulupiriro, anayamba kale kulalikira Uthenga Wabwino kwa Abrahamu, kuti, Idzadalitsidwa mwa iwe mitundu yonse.

9 Kotero kuti iwo a cikhulupiriro adalitsidwa pamodzi ndi Abrahamu wokhulupirikayo,

10 Pakuti onse amene atama nchito za lamulo Iiwakhalira temberero; pakuti kwalembedwa, Wotembereredwa ali yense wosakhala m'zonse zolembedwa m'buku la cilamulo, kuzicita izi.

11 Ndipo cidziwikatu kuti palibe munthu ayesedwa wolungama ndi lamulo pamaso pa Mulungu; pakuti, Wolungama adzakhala ndi moyo ndi cikhulupiriro;

12 koma cilamulo sicicokera kucikhulupiriro; koma, Wakuzicita izi adzakhala ndi moyo ndi izi.

13 Kristu anatiombola ku temberero la cilamulo, atakhala temberero m'malo mwathu; pakuti kwalembedwa, Wotembereredwa ali yense woo paeikidwa pamtengo;

14 kutidalitso la Abrahamu mwa Yesu Kristu, licitike kwa amitundu; kuti tikalandire lonjezano la Mzimuyo, mwa cikhulupiriro.

15 Abale, ndinena monga munthu Pangano, lingakhale la munthu, litalunzika, palibe munthu aliyesacabe, kapena kuonjezapo.

16 Ndipo malonjezano ananenedwa kwa Abrahamu ndi kwa mbeu yace, Sanena, Ndipo kwa zimbeu, ngati kunena zambiri; komatu ngati kunena imodzi, Ndipo kwa mbeu yako, ndiye Kristu.

17 Ndipo ici ndinena; Lamulo, limene linafika zitapita zaka mazana anai mphambu makumi atatu, silifafaniza pangano lolunzika kale ndi Mulungu, kuliyesa lonjezanolo lacabe.

18 Pakuti ngati kulowa nyumba kucokera kulamulo, sikucokeranso kulonjezano; koma kumeneku Mulungu anampatsa Abrahamu kwaufulu mwa lonjezano.

19 Nanga cilamulo tsono? Cinaoniezeka cifukwa ca zolakwa, kufikira ikadza mbeu imene adailonjezera; ndipo cinakonzeka ndi angelo m'dzanja la Ilkhoswe.

20 Koma nkhoswe siiri ya mmodzi; koma Mulungu ali mmodzi.

21 Pamenepo kodi cilamulo citsutsana nao malonjezano a Mulungu? Msatero ai. Pakuti cikadapatsidwa cilamulo eakukhoza kucitira moyo, cilungamo cikadacokera ndithu kulamulo.

22 Komatu lembo Iinatsekereza zonse pansi pa ucimo, kuti lonjezano la kwa cikhulupiriro ca Yesu Kristu likapatsidwe kwa okhulupirirawo.

23 Koma cisanadze cikhulupiriro tinasungidwa pomvera lamulo otsekedwa kufikira cikhulupiriro cimene cikabvumbulutsidwa bwino bwino.

24 1 Momwemo cilamulo cidakhala namkungwi wathu wakutifikitsa kwa Kristu, 2 kuti tikayesedwe olungama ndi cikhulupiriro.

25 Koma popeza cadza cikhulupiriro, sitikhalanso omvera namkungwi.

26 3 Pakuti inu nonse muli ana a Mulungu, mwa cikhulupiriro ca mwa Yesu Kristu.

27 4 Pakuti nonse amene munabatizidwa kwa Kristu mudabvala Kristu.

28 5 Muno mulibe Myuda, kapena Mhelene, muno mulibe kapolo, kapena mfulu, muno mulibe mwamuna ndi mkazi; 6 pakuti muli nonse mmodzi mwa Kristu Yesu.

29 Koma ngati muli a Kristu, muli mbeu ya Abrahamu, 7 nyumba monga mwa Lonjezano.

4

1 Koma ndinena kuti, pokhala wolowa nyumba ali wakhanda, sasiyana ndi kapolo, angakhale ali mwini zonse;

2 komatu ali wakumvera omsungira ndi adindo, kufikira nthawi yoikika kale ndi atate wace.

3 Koteronso ife, pamene tinali akhanda, tinali akapolo akumvera miyambo ya dziko lapansi;

4 koma pokwaniridwa nthawi, Mulungu anatuma Mwana wace, wobadwa ndi mkazi, wobadwa wakumvera lamulo,

5 kuti akaombole iwo akumvera lamulo, kuti ife tikalandire umwana.

6 Ndipo popeza muli ana, Mulungu anatumiza Mzimu wa Mwana wace alowe m'mitima yathu, wopfuula Abba, Atate.

7 Kotero kuti sulinso kapolo, koma mwana; koma ngati mwana, wolowa nyumbanso mwa Mulungu.

8 Komatu pajapo, posadziwa Mulungu inu, munacitira ukapolo iyo yosakhalamilungu m'cibadwidwe cao;

9 koma tsopano, podziwa Mulungu inu, koma makamaka podziwika ndi Mulungu, mubwereranso bwanji kutsata miyambo yofoka ndi yaumphawi, imene mufuna kubwerezanso kuicitira ukapolo?

10 Musunga masiku, ndi miyezi, ndi nyengo, ndi zaka.

11 Ndiopera inu, kuti kapena odadzibvutitsa ndi inu cabe.

12 Abale, ndikupemphani, khalani monga ine, pakuti inenso ndiri mongainu. Simunandicitira coipa ine;

13 koma mudziwa kuti m'kufoka kwa thupi ndinakulalikirani Uthenga Wabwino poyamba:

14 ndipo cija ca m'thupi langa cakukuyesani inu simunacipeputsa, kapena sicinakunyansirani, komatu munandilandira ine monga mngelo wa Mulungu, monga Kristu Yesu mwini.

15 Pamenepo thamo lanu liri kuti? Pakuti ndikucitirani inu umboni, kuti, kukadatheka, mukadakolowola maso anu ndi kundipatsa ine.

16 Kotero kodi ndasanduka mdani wanu, pakukunenerani zoona?

17 Acita cangu pa inu koma si kokoma ai, komatu afuna kukutsekerezani inu kunja, kuti mukawacitire iwowa cangu.

18 Koma nkwabwino kucita cangu m'zabwino nthawi zonse, si pokha pokha pokhala nanu pamodzi ine.

19 Tiana tanga, amene ndirikumvanso zowawa za kubala inu, kufikira Kristu aumbika mwa inu,

20 koma mwenzi nditakhala nanu tsopano, ndi kusintha mau anga; cifukwa ndisinkhasinkha nanu.

21 Ndiuzeni, inu akufuna kukhala omvera lamulo, kodi simukumva cilamulo?

22 Pakuti palembedwa, kuti Abrahamu anali nao ana amuna awiri, mmodzi wobadwa mwa mdzakazi, ndi mmodzi wobadwa mwa mfulu.

23 Komatu uyo wa mdzakazi anabadwa monga mwa thupi; koma iye wa mfuluyo, anabadwa monga mwa Ionjezano, Izo ndizo zophiphiritsa;

24 pakuti akaziwa ali mapangano awiri, mmodzi wa ku phiri la Sinai, akubalira ukapolo, ndiye Hagara.

25 Koma Hagara ndiye phiri la Sinai, m'Arabiya, nafanana ndi Yerusalemu wa tsopano; pakuti ali muukapolo pamodzi ndi ana ace.

26 Koma, Yerusalemu wa kumwamba uli waufulu, ndiwo amai wathu.

27 Pakuti kwalembedwa, Kondwera, cumba iwe wosabala; Yimba nthungululu, nupfuule iwe wosamva kuwawa kwa kubala; Pakuti ana ace a iye ali mbeta acuruka koposa ana a iye ali naye mwamuna.

28 Koma ife, abale, monga Isake, tiri ana a lonjezano.

29 Komatu monga pompaja iye wobadwa monga mwa thupi anazunza wobadwa monga mwa Mzimu, momwemonso tsopano,

30 Koma lembo linena ciani? Taya kubwalo mdzakazi ndi mwana wace, pakuti sadzalowa nyumba mwanawa mdzakazi pamodzi ndi mwana wa mfulu.

31 Cifukwa cace, abale, z sitiri ana a mdzakazi, komatu a mfulu.

5

1 Kristu anatisandutsa mfulu, kuti tikhale mfulu; cifukwa cace cirimikani, musakodwenso ndi gori la ukapolo.

2 Taonani, ine Paulo ndinena ndi inu, kuti, ngati mulola akuduleni, Kristu simudzapindula naye kanthu.

3 Ndicitanso umboni kwa munthu yense wolola amdule, kuti ali wamangawa kucita cilamulo conse.

4 Mulibe kanthu ndi Kristu, inu amene muyesedwa olungama ndi lamulo; mudagwa posiyana naco cisomo.

5 Pakuti ife mwa Mzimu, kucokera m'cikhulupiriro, tilindira ciyembekezo ca cilungamo,

6 Pakuti mwa Kristu Yesu kapena mdulidwe kapena kusadulidwa kulibe mphamvu; komatu cikhulupiriro cakucititsa mwa cikondi.

7 Munathamanga bwino; anakuletsani ndani kuti musamvere coonadi?

8 Kukopa kumene sikucokera kwa iye anakuitanani.

9 Cotupitsa pang'ono citupitsa mtanda wonse.

10 Ine ndikhulupirira inu mwa Ambuye, kuti simudzakhala nao mtima wina; koma iye wakubvuta inu, angakhale ali yani, adzasenza citsutso cace.

11 Koma ine, abale, ngati ndilalikiransoindulidwe, ndizunzikanso bwanji? Pamenepo cikhumudwitso ca mtanda cidatha.

12 Mwenzi atadzidula, iwo akugwedezetsani inu.

13 Pakuti adakuitanani inu, abale, mukhale mfulu; cokhaco musacite nao ufulu wanu cothandizira thupi, komatu mwa cikondi citiranani ukapolo.

14 Pakuti mau amodzi akwaniritsa cilamulo conse ndiwo; Uzikonda mnzako monga udzikonda iwe mwini.

15 Koma ngati mulumana ndi kudyana, cenjerani mungaonongane.

16 Koma ndinena, Muyendeyende ndi Mzimu, ndipo musafitse cilakolako ca thupi.

17 Pakuti thupi lilakalaka potsutsana naye Mzimu, ndi Mzimu potsutsana nalo thupi; pakuti izi sizilingana; kuti zimene muzifuna musazicite.

18 Ngati Mzimu akutsogolerani, simuli omvera lamulo.

19 Ndipo nchito za thupi zionekera, ndizo dama, codetsa, kukhumba zonyansa, kupembedza mafano,

20 nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko, njiru,

21 kuledzera, mcezo, ndi zina zotere; zimene ndikucenjezani nazo, monga ndacita, kuti iwo akucitacita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

22 Koma cipatso ca Mzimu ndico cikondi, cimwemwe, mtendere, kuleza mtima, cifundo, kukoma mtima, icikhulupirtro,

23 cifatso, ciletso; pokana zimenezi palibe lamulo.

24 Koma iwo a Kristu Yesu adapacika thupi, ndi zokhumba zace, ndi zilakolako zace.

25 1 N gati tiri ndi moyo ndi Mzimu, ndi Mzimunso tiyende.

26 2 Tisakhale odzikuza, outsana, akucitirana njiru.

6

1 Abale, ngatinso munthu agwidwa nako kulakwa kwakuti, inu auzimu, mubweze wotereyo mu mzimu wa cifatso; ndikudzipenyerera wekha, ungayesedwe nawenso.

2 Nyamuliranani zothodwetsa, ndipo kotero mufitse cilamulo ca Kristu.

3 Pakuti ngati wina ayesa ali kanthu pokhala ali cabe, adzinyenga yekha.

4 Koma yense ayesere nchito yace ya iye yekha, ndipo pamenepo adzakhala nako kudzitamandira cifukwa ca iye yekha, si cifukwa ca wina,

5 Pakuti yense adzasenza katundu wace wa iye mwini.

6 Koma iye amene aphunzira mau, ayenera kucereza womphunzitsayo m'zonse zabwino.

7 Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti cimene munthu acifesa, cimenenso adzacituta.

8 Pakuti wakufesera kwa thupi la iye yekha, cocokera m'thupi adzatuta cibvundi; koma wakufesera kwa Mzimu, cocokera mu Mzimu adzatuta moyo wosatha.

9 Koma tisaleme pakucita zabwino pakuti pa nyengo yace tidzatuta tikapanda kufoka.

10 Cifukwa cace, monga tiri nayo nyengo, ticitire onse cokoma, koma makamaka iwo a pa banja la cikhulupiriro.

11 Taonani, malembedwe akuruwo ndakulemberani inu ndi dzanja langa la ine mwini.

12 Onseamene afuna kuonekera okoma m'thupi, iwowa akukangamizani inu mudulidwe; cokhaco, cakuti angazunzike cifukwa ca mtanda wa Kristu.

13 Pakuti angakhale iwo omwe odulidwa sasunga lamulo; komatu afuna inu mudulidwe, kuti akadzitamandire m'thupi lanu.

14 Koma kudzitamandira ine konse konse, iai, koma mu mtanda wa Ambuye wathu Yesu Kristu, amene mwa iye dziko lapansi lapacikidwira ine, ndi ine ndapacikidwira dziko lapansi.

15 Pakuti mdulidwe ulibe kanthu, kusadulidwakulibe kanthunso, komatu wolengedwa watsopano.

16 Ndipo onse amene atsatsa cilangizo ici, mtendere ndi cifundo zikhale pa iwo, ndi pa Israyeli wa Mulungu.

17 Kuyambira tsopano palibe munthu andibvute, pakuti ndiri nayo ine m'thupi mwanga mikwingwirima ya Yesu.

18 Cisomo ca Ambuye wathu Yesu Kristu cikhale ndi mzimu wanu, abale. Amen.