1 NDIPO Yehova anaitana Mose, nanena naye ali m'cihema cokomanako iye, nati,
2 Lankhula ndi ana a lsrayeli, nunene nao, Ali yense mwa inu akabwera naco copereka ca kwa Yehova, muzibwera naco copereka canu cikhale ca zoweta, ca ng'ombe, kapena ca nkhosa, kapena ca mbuzi.
3 Copereka cace cikakhala nsembe yopsereza ya ng'ombe, azibwera nayo yaimuna yopanda cirema; abwere nayo ku khomo la cihema cokomanako, kuti alandirike pamaso pa Yehova.
4 Ndipo aike dzanja lace pamutu pa nsembe yopsereza; ndipo idzalandiridwa m'malo mwace, imtetezere.
5 Pamenepo aiphe ng'ombeyo pamaso pa Yehova; ndipo ana a Aroni, ansembewo, abwere nao mwazi, nawaze mwaziwo pozungulira pa guwa la nsembe, lokhala pa khoma la cihema cokomanako.
6 Ndipo asende nsembe yopsereza, ndi kuikadzula ziwalo zace.
7 Ndipo ana a Aroni asonkhe mota pa guwa la nsembe, ndi kukonza nkhuni pamotopo;
8 ndi ana a Aroni, ansembewo, akonze ziwalozo, mutu, ndi mafuta pa nkhuni ziri pa mota wa pa guwa la nsembe;
9 koma atsuke ndi madzi matumbo ace ndi miyendo yace; ndi wansembe atenthe zonsezi pa guwa la nsembe, zikhale nsembe yopsereza, nsembe yamoto, ya pfungo lokoma la kwa Yehova.
10 Ndipo copereka cace cikakhala ca nkhosa, kapena ca mbuzi, cikhale nsembe yopsereza; azibwera nayo yaimuna yopanda cirema.
11 Ndipo aiphere iyo pa mbali ya kumpoto ya guwa la nsembe, pamaso pa Yehova; ndipo ana a Aroni, ansembewo, awaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.
12 Ndipo aikadzule ziwalo zace, pamodzi ndi mutu wace ndi mafuta ace; ndi wansembeyo akonze izi pa nkhuni ziri pa mota wa pa guwa la nsembe.
13 Koma atsuke ndi madzi matumbo ndi miyendo; ndi wansembe abwere nazo zonse nazitenthe pa guwa la nsembe; ndiyo nsembe yopsereza, nsembe yamoto, ya pfungo lokoma la kwa Yehova.
14 Ndipo copereka cace ca kwa Yehova cikakhala nsembe yopsereza ya mbalame, azibwera naco copereka cace cikhale ca njiwa, kapena ca maunda.
15 Ndipo wansembe abwere naco ku guwa la nsembe, namwetule mutu wace, naitenthe pa guwa la nsembe; ndi mwazi wace aukamulire pa mbali ya guwa la nsembe,
16 nacotse citsokomero, ndi cipwidza cace, nazitaye kufupi kwa guwa la nsembe, kum'mawa, kudzala;
17 nang'ambe mapiko ace osawacotsa konse ai; ndipo wansembeyo aitenthe pa guwa la nsembe, pa nkhuni ziri pamoto; ndiyo nsembe yopsereza, nsembe yamoto, ya pfungo lokoma la kwa Yehova.
1 Ndipo munthu akabwera naco copereka ndico nsembe yaufa ya kwa Yehova, copereka cace cizikhala ca ufa wosalala; ndipo athirepo mafuta, ndi kuikapo libano.
2 Ndipo abwere nayo kwa ana a Aroni, ansembewo; natengeko ufa, ndi mafuta odzala manja, ndi libano wace wonse; ndipo wansembeyo aitenthe cikumbutso cace pa guwa la nsembe, ndiyo nsembe yamoto, ya pfungo lokoma la kwa Yehova.
3 Ndipo cotsalira ca nsembe yaufa cikhale ca Aroni ndi ana ace; ndico copatulikitsa ca nsembe zamoto za Yehova.
4 Ndipo ukabwera naco copereka ndico nsembe yaufa, yophika mumcembo, cizikhala ca timitanda ta ufa wosalala topanda cotupitsa tosanganiza ndi mafuta, kapena timitanda taphanthi topanda cotupitsa todzoza ndi mafuta.
5 Ndipo nsembe yaufa yako ikakhala yokazinga m'ciwaya, ikhale ya ufa wosalala wopanda cotupitsa, wosanganiza ndi mafuta.
6 Uphwanye, nuthirepo mafuta; ndiyo nsembe yaufa.
7 Ndipo copereka cako cikakhala nsembe yaufa ya mumphika, cikhale ca ufa wosalala ndi mafuta.
8 Ndipo ubwere nayo nsembe yaufa yopangika ndi izi kwa Yehova; ndipo atabwera naco kwa wansembe, iyeyo apite naco ku guwa la nsembe.
9 Ndipo wansembeyo atengeko cikumbutso pa nsembe yaufa, nacitenthe pa guwa la nsembe; ndico nsembe yamoto ya pfungo lokoma la kwa Yehova.
10 Ndipo cotsalira ca nsembe yaufa cikhale ca Aroni ndi ana ace; ndico copatulikitsa ca nsembe zamoto za Yehova.
11 Nsembe iri yonse yaufa, imene mubwera nayo kwa Yehova, isapangike ndi cotupitsa, pakuti musamatenthera Yehova nsembe yamoto yacotupitsa, kapena yauci.
12 Monga copereka ca zipatso zoyamba muzipereka izi: koma asazifukize pa guwa la nsembe zicite pfungo lokoma.
13 Ndipo copereka cako ciri conse ca nsembe yaufa uzicikoleretsa ndi mcere; usasowe mcere wa cipangano ca Mulungu wako pa nsembe yako yaufa; pa zopereka zako zonse uzipereka mcere.
14 Ndipo ukabwera nayo nsembe yaufa ya zipatso zoyamba kwa Yehova, uzibwera nayo nsembe yako ya zipatso zoyamba ikhale ya ngala zoyamba kuca, zoumika pamoto, zokonola.
15 Ndipo uthirepo mafuta, ndi kuikapo libona; ndiyo nsembe yaufa.
16 Ndipo wansembe atenthe cikumbutso cace, atatapa pa tirigu wace wokonola, ndi pa mafuta ace, ndi kutenga libano lace lonse; ndiyo nsembe yamoto ya kwa Yehova.
1 Ndipo copereka cace cikakhala nsembe yoyamika; akabwera nayo ng'ombe, kapena yaimuna kapena yaikazi, azibwera nayo yopanda cirema pamaso pa Yehova.
2 Ndipo aike dzanja lace pa mutu wa copereka cace, ndi kuipha pa cipata ca cihema cokomanako; ndipo ana a Aroni, ansembewo, awaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.
3 Pamenepo abwere nayo nsembe yamoto ya kwa Yehova, yotengako ku nsembe yoyamika; acotse mafuta akukuta matumbo, ndi mafuta onse akukhala pamatumbo,
4 ndi imso ziwiri, ndi mafuta ali pomwepo okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso.
5 Ndipo ana a Aroni azitenthe pa guwa la nsembe, pa nsembe yopsereza, iri pa nkhuni zimene ziri pamoto; ndiyo nsembe yamoto, ya pfungo lokoma la kwa Yehova.
6 Ndipo copereka cace cikakhala nkhosa kapena mbuzi, kuti ikhale nsembe yoyamika ya kwa Yehova; ingakhale yaimuna kapena yaikazi, azibwera nayo yopanda cirema;
7 akabwera nayo nkhosa kuti ikhale copereka cace, abwere nayo pamaso pa Yehova;
8 naike dzanja lace pamutu pa copereka cace, naiphe patsogolo pa cihema cokomanako; ndipo ana a Aroni awaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.
9 Pamenepo abwere nayo nsembe yamoto ya kwa Yehova; yotengako ku nsembe yoyamika; mafuta ace, mcira wamafuta wonse, ataucotsa kufupi ku pfupa lao msana; naicotse mafuta akukuta matumbo, ndi mafuta onse akukhala pamatumbo,
10 ndi imso ziwiri, ndi mafuta ali pomwepo, okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso.
11 Ndipo wansembe azitenthe pa guwa la nsembe; ndico cakudya ca nsembe yamoto ya kwa Mulungu.
12 Ndipo copereka cace cikakhala mbuzi, azibwera nayo pamaso pa Yehova;
13 naike dzanja lace pamutu pace, naiphe pa khomo la cihema cokomanako; ndipo ana a Aroni awaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.
14 Ndipo abwere naco copereka cace cotengako, ndico nsembe yamoto ya kwa Yehova; acotse mafuta akukuta matumbo, ndi mafuta onse akukhala pamatumbo,
15 ndi imso ziwiri, ndi mafuta ali pomwepo, okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso.
16 Ndipo wansembe atenthe izi pa guwa la nsembe; ndizo cakudya ca nsembe yamoto icite pfungo lokoma; mafuta onse nga Yehova.
17 Likhale lemba losatha m'mibadwo yanu m'nyumba zanu zonse, musamadya kapena mafuta kapena mwazi.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2 Lankhula ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Munthu akacimwa, osati dala, pa cina ca zinthu ziri zonse aziletsa Mulungu, nakacitapo kanthu;
3 akalakwa wansembe wodzozedwa ndi kuparamulira anthu; pamenepo azibwera nayo kwa Yehova ng'ombe yamphongo, yopanda cirema, cifukwa ca kucimwa kwace adakucita, ikhale nsembe yaucimo.
4 Ndipo adze nayo ng'ombeyo ku khomo la cihema cokomanako pamaso pa Yehova; naike dzanja lace pamutu pa ng'ombeyo, naiphe ng'ombeyo pamaso pa Yehova.
5 Ndipo wansembe wodzozedwayo atengeko mwazi wa ng'ombeyo, nabwerenao ku cihema cokomanako;
6 ndipo wansembeyo abviike cala cace m'mwazimo, nawaze mwaziwo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova cakuno ca nsaru yocinga, ya malo opatulika.
7 Ndipo wansembeyo atengeko mwazi, nauike pa nyanga za guwa la nsembe la cofukiza ca pfungo lokoma, lokhala m'cihema cokomanako pamaso pa Yehova; nathire mwazi wonse wa ng'ombeyo patsinde pa guwa la nsembe yopsereza, lokhala pa khomo la cihema cokomanako.
8 Ndipo acotse mafuta onse a ng'ombe ya nsembe yaucimo, acotse mafuta akukuta matumbo, ndi mafuta onse akukhala pamatumbo,
9 ndi imso ziwiri ndi mafuta ali pomwepo, okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso,
10 umo azikacotsera pa ng'ombe ya nsembe yoyamika; ndipo wansembe azitenthe pa guwa la nsembe yopsereza.
11 Naturutse cikopa ca ng'ombeyo, ndi nyama yace yonse, pamodzi ndi mutu wace, ndi miyendo yace, ndi matumbo ace, ndi cipwidza cace,
12 inde ng'ombe yonse, kunja kwa cigono, kumka nayo kumalo koyera, kumene atayako mapulusa, naitenthe pankhuni ndi moto; aitenthe potayira mapulusa.
13 Ndipo khamu lonse la Israyeli likalakwa osati dala, ndipo cikabisika cinthuci pamaso pa msonkhano, litacita cina ca zinthu ziri zonse aziletsa Yehova, ndi kuparamula;
14 kukadziwika kucimwa adacimwako, pamenepo msonkhano uzibwera nayo ng'ombe yamphongo, ikhale nsembe yaucimo, ndipo udze nayo ku khomo la cihema cokomanako.
15 Ndipo akuru a khamulo aike manja ao pamutu pa ng'ombeyo, pamaso pa Yehova; naiphe ng'ombeyo pamaso pa Yehova.
16 Ndipo wansembe wodzozedwayo adze nao mwazi wina wa ng'ombeyo ku cihema cokomanako;
17 nabviike cala cace m'mwazi wa nsembewo, nauwaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, cakuno ca nsaru yocinga.
18 Naike mwazi wina pa nyanga za guwa la nsembe, lokhala pamaso pa Yehova, lokhala m'cihema cokomanako; nathire mwazi wonse patsinde pa guwa la nsembe yopsereza, lokhala pa khomo la cihema cokomanako.
19 Ndipo acotse mafuta ace onse, nawatenthe pa guwa la nsembe.
20 Atero nayo ng'ombeyo; monga umo anacitira ng'ombe ya nsembe yaucimo; ndipo wansembe awacitire cowatetezera, ndipo adzakhululukidwa.
21 Ndipo aturutse ng'ombeyo kunja kwa cigono, ndi kuitentha monga anatenthera ng'ombe yoyamba ija; ndiyo nsembe yaucimo ya kwa msonkhano.
22 Akacimwa mkuru, osati dala, pa cina ca zinthu ziti zonse aziletsa Yehova Mulungu wace, naparamula;
23 akamdziwitsa kucimwa kwace adacimwako, azidza naco copereka cace, ndico tonde wopanda cirema;
24 naike dzanja lace pamutu pa mbuziyo, naiphe pamalo pophera nsembe yopsereza pamaso pa Yehova; ndiyo nsembe yaucimo.
25 Ndipo wansembe atengeko mwazi wa nsembe yaucimo ndi cala cace, nauike pa nyanga za guwa la nsembe yopsereza, ndi kuthira mwazi wace patsinde pa guwa la nsembe yopsereza.
26 Ndipo atenthe mafuta ace onse pa guwa la nsembe, monga mafuta a nsembe yoyamika; ndipo wansembe amcitire comtetezera, ndipo adzakhululukidwa.
27 Ndipo akacimwa wina wa anthu a m'dziko, osati dala, pa cina ca zinthu ziri zonse aziletsa Yehova, naparamula;
28 akamdziwitsa kucimwa kwace adacimwako, azidza naco copereka cace mbuzi yaikazi, yopanda cirema, cifukwa ca kucimwa kwace adakucita.
29 Aike dzanja lace pamutu pa nsembe yaucimo, naiphe nsembe yaucimo pamalo pa nsembe yopsereza.
30 Ndipo wansembe atengeko mwazi ndi cala cace, nauike pa nyanga za guwa la nsembe yopsereza, ndi kuthira mwazi wace wonse patsinde pa guwa la nsembe.
31 Nacotse mafuta ace onse, monga umo amacotsera mafuta pa nsembe yoyamika; ndipo wansembeyo awatenthe pa guwa la nsembe akhale pfungo lokoma la kwa Yehova; ndi wansembe amcitire comtetezera, ndipo adzakhululukidwa.
32 Ndipo akadza nayo nkhosa, ndiyo copereka cace, ikhale nsembe yaucimo, azidza nayo yaikazi, yopanda cirema.
33 Naike dzanja lace pa mutu wa nsembe yaucimo, ndi kuipha ikhale nsembe yaucimo pamalo pophera nsembe yopsereza.
34 Ndipo wansembe atengeko mwazi wa nsembe yaucimo ndi cala cace, nauike pa nyanga za guwa la nsembe yopsereza, ndi kuthira mwazi wace wonse patsinde pa guwa la nsembe;
35 nawacotse mafuta ace onse, monga umo amacotsera mafuta a nkhosa pa nsembe yoyamika; ndipo wansembeyo atenthe, awa pa guwa la nsembe, monga umo amacitira nsembe zamoto za Yehova; ndipo wansembeyo amcitire comtetezera pa kucimwa kwace adakucimwira, ndipo adzakhululukidwa.
1 Ndipo akacimwa munthu, wakuti adamva mau akuwalumbiritsa, ndiye mboni, kapena wakuona, kapena wakudziwa, koma osaulula, azisenza mphulupulu yace;
2 kapena munthu akakhudza ciri conse codetsa kapena mtembo wa nyama yodetsa, kapena mtembo wa coweta codetsa, kapena mtembo wa cokwawa codetsa, kungakhale kudambisikira, ali wodetsedwa, ndi woparamula.
3 Kapena akakhudza codetsa ca munthu, ndico codetsa ciri conse akakhala codetsedwa naco, ndipo cidambisikira; koma pocizindikira akhala woparamula:
4 kapena munthu akalumbira ndi milomo yace osalingirira kucita coipa, kapena kucita cabwino, ciri conse munthu akalumbira osalingirira, ndipo cidambisikira; koma pocizindikira akhala woparamula cimodzi ca izi:
5 ndipo kudzali, ataparamula cimodzi ca izi, aziulula cimene adacimwa naco;
6 nadze nayo nsembe yoparamula kwa Yehova cifukwa ca kulakwa kwace adacimwira, ndiyo msoti wa nkhosa, kapena msoti wa mbuzi, ukhale nsembe yaucimo; ndipo wansembe amcitire comtetezera cifukwa ca kucimwa kwace.
7 Ndipo cuma cace cikapanda kufikira nkhosa, wocimwayo adze nayo kwa Yehova nsembe yace yoparamula, njiwa ziwiri, kapena maunda awiri; imodzi ikhale ya nsembe yaucimo, ndi yina ya nsembe yopsereza.
8 Ndipo adze nazo kwa wansembe, ndiye ayambe kubwera nayo ija ya kwa nsembe yaucimo, napotole mutu wace pakhosi pace, osaucotsa;
9 nawazeko mwazi wa nsembe yaucimo pa mbali ya guwa la nsembe; ndi mwazi wotsalira aukamulire patsinde pa guwa la nsembe; ndiyo nsembe yaucimo.
10 Ndipo aikonze inzace ikhale nsembe yopsereza, manga mwa lemba lace; ndipo wansembe amcitire comtetezera cifukwa ca kucimwa adacimwira, ndipo adzakhululukidwa.
11 Koma cuma cace cikapanda kufikira njiwa ziwiri kapena maunda awiri, wocimwayo azidza naco copereka cace limodzi la magawo khumi la efa la ufa wosalala, likhale la nsembe yaucima; asamaikapo mafuta, kapena kuikapo libona ai; pakuti ndico nsembe yaucimo.
12 Ndipo adze naco kwa wansembe, ndi wansembeyo atengeko wodzala manja ukhale cikumbutso cace, nacitenthe pa guwa la nsembe monga umo amacitira nsembe zamoto za Yehova; ndiyo nsembe yaucimo.
13 Ndipo wansembe amcitire comtetezera cifukwa ca kucimwa kwace adacimwira cimodzi ca izi, ndipo adzakhululukidwa; ndipo cotsalira cikhale ca wansembe, monga umo amacitira copereka caufaco.
14 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
15 Munthu akacita mosakhulupirika, nakacimwa osati dala, pa zopatulika za Yehova, azidza nayo nsembe yace yoparamula kwa Yehova, ndiyo nkhosa yamphongo yopanda cirema, ya m'gulu lace, monga umayesa mtengo wace pochula masekeli a siliva, kunena sekeli wa malo opatulika, ikhale nsembe yoparamula;
16 ndipo abwezere colakwira copatulikaco, naonjezepo limodzi la magawo asanu, napereke kwa wansembe; ndi wansembeyo amcitire comtetezera ndi nkhosa yamphongo ya nsembe yoparamula; ndipo adzakhululukidwa.
17 Ndipo munthu akacimwa, nakacita dna ca zinthu ziti zonse aziletsa Yehova; angakhale analibe kudziwa, koma waparamula, azisenza mphulupulu yace.
18 Nadze nayo kwa wansembe nkhosa yamphongo yopanda cirema ya m'khola lace, monga umayesa mtengo wace, ikhale nsembe yoparamula; ndipo wansembeyo amcitire comtetezera cifukwa ca kusacimwa dala kwace, osakudziwa; ndipo adzakhululukidwa.
19 Iyo ndiyo nsembe yoparamula; munthuyu anaparamula ndithu pamaso pa Yehova.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2 Akacimwa munthu nakacita mosakhulupirika pa Yehova nakacita monyenga ndi mnansi wace kunenaza coikiza, kapena cikole, kapena cifwamba, kapena anasautsa mnansi wace;
3 kapena anapeza cinthu cotayika, nanenapo bodza, nalumbira pabodza; pa cimodzi ca izi zonse amacita munthu, ndi kucimwapo;
4 pamenepo padzali kuti popeza anacimwa, naparamula, azibweza zofunkha zimene analanda mwacifwamba, kapena cinthuci adaciona ndi kusautsa mnzace, kapena coikiza anamuikiza, kapena cinthu cotayika anacipeza;
5 kapena ciri conse analumbirapo monama; acibwezere conseci, naonjezepo, limodzi la magawo asanu; apereke ici kwa mwini wace tsiku lotsutsidwa iye.
6 Ndipo adze nayo nsembe yace yoparamula kwa Yehova, ndiyo nkhosa yamphongo yopanda cirema ya m'khola mwace, monga umayesa mtengo wace, ikhale nsembe yoparamula, adze nayo kwa wansembe;
7 ndipo wansembeyo amcitire comtetezera pamaso pa Yehova, ndipo adzakhululukidwa; kunena ziti zonse akazicita ndi kuparamula nazo.
8 Ndipo Yehova analankhula ndi Mose, nati,
9 Uza Aroni ndi ana ace, ndi kuti, Cilamulo ca nsembe yopsereza ndi ici: nsembe yopsereza izikhala pa nkhuni za pa guwa la nsembe usiku wonse kufikira m'mawa; ndipo mota wa pa guwa la nsembe uziyakabe pamenepo.
10 Ndipo wansembe abvale mwinjiro wace wabafuta, nabvale pathupi pace zobvala za pamiyendo zabafuta; naole phulusa, mota utanyeketsa nsembe yamoto pa guwa la nsembe, nalitaye m'mphepete mwa guwa la nsembe.
11 Pamenepo abvule zobvala zace, nabvale zobvala zina, nacotse phulusa kumka nalo kunja kwa cigono, kumalo koyera.
12 Ndipo mota wa pa guwa la nsembe uyakebe pamenepo, wosazima; wansembe ayatsepo nkhuni m'mawa ndi m'mawa; nakonzepo nsembe yopsereza, natenthepo mafuta a nsembe zoyamika.
13 Moto uziyakabe pa guwa la nsembe, wosazima.
14 Ndipo cilamulo ca copereka caufa ndico: ana a Aroni azibwera naco pamaso pa Yehova ku guwa la nsembe.
15 Ndipo atengeko wodzala manja pa ufa wa copereka ca ufa wosalala, ndi pa mafuta ace, ndi libona lonse liri pa copereka caufa, nazitenthe pa guwa la nsembe, zicite pfungo lokoma, ndizo cikumbutso cace ca kwa Yehova.
16 Ndipo cotsalira cace adye Aroni ndi ana ace; acidye copanda cotupitsa m'malo opatulika; pa bwalo la cihema cokomanako acidye.
17 Asaciphike ndi cotupitsa, Ndacipereka cikhale gawo lao locokera pa nsembe zanga zamoto; ndico copatulikitsa, monga nsembe yaucimo, ndi monga nsembe yoparamula.
18 Amuna onse a mwa ana a Aroni adyeko, ndilo lemba losatha la ku mibadwo yanu, ciwacokere ku nsembe zamoto za Yehova; ali yense wakuzikhudza izi adzakhala wapatolika.
19 Ndipo Yehova analankhula ndi Mose, nati,
20 Copereka ca Aroni ndi ana ace, cimene azibwera naco kwa Yehova tsiku la kudzozedwa iye ndi ici: limodzi la magawo khumi la efa la ufa wosalala, likhale copereka caufa kosalekeza, nusu lace m'mawa, nusu lace madzulo.
21 Cikonzeke paciwaya ndi mafuta; udze naco cokazinga; copereka caufa cazidutsu ubwere naco, cikhale pfungo lokoma la kwa Yehova.
22 Ndipo wansembe wodzozedwa m'malo mwace, wa mwa ana ace, acite ici; likhale lemba losatha; acitenthe konse kwa Yehova.
23 Ndipo zopereka zaufa zonse za wansembe azitenthe konse; asamazidya.
24 Ndipo Yehova analankhula ndi Mose, nati,
25 Lankhula ndi Aroni ndi ana ace, ndi kuti, Cilamulo ca nsembe yaucimo ndi ici: Pamalo pophera nsembe yopsereza ndipo pophera nsembe yaucimo pamaso pa Yehova; ndiyo yopatulikitsa.
26 Ndipo azidya iyi wansembe amene aipereka cifukwa ca zoipa; aidyere m'malo opatulika, pa bwalo la cihema cokomanako.
27 Ali yense akakhudza nyama yace adzakhala wopatulika; ndipo akawaza mwazi wace wina pa cobvala ciri conse, utsuke cimene adauwazaco m'malo opatulika.
28 Ndipo mphika wadothi umene anaphikamo nyamayi auswe, koma ngati anaiphika mu mphika wamkuwa, atsuke uwu, nautsukuluze ndi madzi.
29 Amuna onse a mwa ansembe adyeko; ndiyo yopatulikitsa.
30 Koma asadye nsembe yaucimo iri yonse, imene amadza nao mwazi wace ku cihema cokomanako kutetezera nao m'malo opatulika; aitenthe ndi moto.
1 Ndipo cilamulo ca nsembe yoparamula ndi ici: ndiyo yopatulikitsa.
2 Pamalo pophera nsembe yopsereza ndipo aziphera nsembe yoparamula; nawaze mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.
3 Ndipo acotseko, nabwere nao mafuta ace onse; mcira wamafuta, ndi mafuta akukuta matumbo,
4 ndi imso ziwiri, ndi mafuta a pamenepo, okhala m'cuuno, ndi cokuta ca mphafa cofikira kuimso;
5 ndipo wansembe atenthe izi pa guwa la nsembe, nsembe yamoto ya kwa Yehova; ndiyo nsembe yoparamula.
6 Amuna onse a mwa ansembe adyeko; adyere m'malo opatulika; ndiyo yopatulikitsa.
7 Monga nsembe yaucimo, momwemo nsembe yoparamula; pa zonse ziwirizi pali cilamulo cimodzi; ikhale yace ya wansembeyo, amene acita nayo cotetezera.
8 Ndipo cikopa ca nsembe yopsereza cikhale cace cace ca wansembe, amene anabwera nayo nsembe yopsereza ya munthu ali yense.
9 Ndipo nsembe zaufa zonse zophika mumcembo, ndi zonse zokonzeka mumphika, ndi paciwaya, zikhale za wansembe amene wabwera nazo,
10 Ndipo nsembe zonse zaufa zosanganiza ndi mafuta, kapena zouma zikhale za ana onse a Aroni, alandireko onse.
11 Ndipo cilamulo ca nsembe zoyamika, zimene azibwera Daze kwa Yehova ndi ici:
12 akabwera nayo kuti ikhale nsembe yolemekeza, azibwera nato, pamodzi ndinsembe yolemekeza, timitanda topanda cotupitsa tosanganiza ndi mafuta, ndi timitanda taphanthi topanda cotupitsa todzoza ndi mafuta, ndi timitanda tooca, ta ufa wosalala tosanganiza ndi mafuta.
13 Abwere naco copereka cace pamodzi ndi timitanda ta mkate wacotupitsa, pamodzi ndi nsembe yolemekeza, ya nsembe zoyamika zace.
14 Ndipo pa zopereka zonsezi atengepo ndi kubwera nako kamtanda kamodzi, kuti kakhale ka nsembe yokweza ya kwa Yehova; kakhale ka wansembe wakuwaza mwazi wa nsembe zoyamika.
15 Kunena za nyama ya nsembe volemekeza ya nsembe zoyamika zace, aziidya tsiku lomwelo lakuipereka; asasiyeko kufikira m'mawa.
16 Koma nsembe ya copereka cace ikakhala ya cowinda, kapena copereka caufuhi, aidye tsiku lomwelo anabwera nayo nsembe yace; ndipo m'mawa adye cotsalirapo;
17 koma cotsalira pa nyama ya nsembeyo tsiku lacitatu, acitenthe.
18 Ndipo akadyako nyama ya nsembe zoyamika zace tsiku lacitatu, sikubvomerezeka kumene; sadzamwerengera wobwera nayo; ndiyo cinthu conyansa, ndipo munthu wakudyako adzasenza mphulupulu zace.
19 Ndipo nyama yokhudza kanthu kali konse kodetsa isadyeke; aitenthe ndi moto. Koma za nyama yina, ali yense ayera aidyeko.
20 Koma munthu akadya nyama ya nsembe zoyamika za Yehova, pokhala naco comdetsa, munthuyo asadzidwe kwa anthu a mtundu wace.
21 Ndipo munthu akakhudza cinthu codetsa, codetsa ca munthu, kapena codetsa ca zoweta, kapena ciri conse conyansa codetsa, nakadyako nyama ya nsembe zoyamika za Yehova, munthuyo asadzidwe kwa anthu a mtundu wace.
22 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
23 Lankhula ndi ana a Israyeli ndi kuti, Musamadya mafuta ali onse, a ng'ombe, kapena a nkhosa, kapena a mbuzi.
24 Ndipo mafuta a iyo idafa yokha, ndi mafuta a iyo idajiwa ndi cirombo ayenera nchito iri yonse, koma musamadya awa konse konse.
25 Pakuti ali yense akadya mafuta a nyama imene amabwera nayo ikhale nsembe yamoto ya kwa Yehova, munthu amene akadya awa asadzidwe kwa anthu a mtundu wace.
26 Ndipo musamadya mwazi uti wonse, kapena wa mbalame, kapena wa nyama, m'nyumba zanu zonse,
27 Ali yense akadya mwazi uti wonse, munthuyo asadzidwe kwa anthu a mtundu wace.
28 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
29 Lankhula ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Wakubwera nayo nsembe yoyamika yace kwa Yehova, azidza naco copereka cace kwa Yehova cocokera ku nsembe yoyamika yace;
30 adze nazo m'manja mwace nsembe zamoto za Yehova; adze nao mafuta pamodzi ndi nganga, kuti aweyule ngangayo ikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
31 Ndipo wansembeyo atenthe mafutawo pa guwa la nsembe; koma ngangayo ikhale ya Arent ndi ana ace.
32 Ndipo mwendo wathako wa ku dzanja lamanja muupereke kwa wansembe, ukhale nsembe yokweza yocokera ku nsembe zoyamika zanu.
33 Mwendo wathako wa ku dzanja lamanja ukhale gawo lace la iyeyu mwa ana a Aroni wakubwera Ilao mwazi wa zopereka zoyamika, ndi mafuta.
34 Pakuti ndatengako kwa ana a Israyeli, ku nsembe zoyamika zao, nganga ya nsembe yoweyula, ndi mwendo wathako wa ku dzanja lamanja wa nsembe yokweza; ndipo ndazipereka kwa Aroni wansembe ndi kwa ana ace, zikhale zoyenera iwo kosatha zocokera kwa ana a Israyeli.
35 Ili ndi gawo la Aroni, ndi gawo la ana ace, locokera ku nsembe zamoto za Yehova, analinena, tsiku limene iye anawasendeza alowe utumiki wa ansembe a Yehova;
36 limene Yehova anauza ana a Israyeli aziwapatsa, tsiku limene iye anawadzoza. Likhale lemba losatha mwa mibadwo yao.
37 Ico ndi cilamulo ca nsembe yopsereza, ca nsembe yaufa, ca nsembe yaucimo, ndi ca nsembe yoparamula, ndi ca kudzaza dzanja, ndi ca nsembe zoyamika;
38 cimene Yehova analamulira Mose m'phiri la Sinai, tsikuli anauza ana a Israyeli abwere nazo zopereka zao kwa Yehova, m'cipululu ca Sinai.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2 Tenga Aroni ndi ana ace pamodzi naye ndi zobvalazo, ndi mafuta odzozawo, ndi ng'ombe ya nsembe yaucimoyo, ndi nkhosa zamphongo ziwirizo, ndi mtanga wa mkate wopanda cotupitsawo;
3 nusonkhanitse khamu lonse ku khomo la cihema cokomanako.
4 Ndipo Mose anacita monga Yehova anamuuza; ndi khamulo linasonkhana pa khomo la cihema cokomanako.
5 Ndipo Mose anati kwa msonkhanowo, Ici ndi cimene Yehova adauza kuti cicitike.
6 Ndipo Mose anabwera nao Aroni ndi ana ace, nawasambitsa ndi madzi,
7 Ndipo anambveka ndi maraya a m'kati, nammanga m'cuuno ndi mpango, nambveka ndi mwinjiro, nambveka ndi efodi, nammanga m'cuuno ndi mpango wa efodi nammanga nao pathupi pace.
8 Ndipo anamuika capacifuwa; naika m'capacifuwa Urimu ndi Tumimu.
9 Naika nduwirayo pamutu pace; ndi panduwira, pamphumi pace anaika golidi waphanthiphanthi, ndiwo korona wopatulika; monga Yehova adauza Mose.
10 Ndipo Mose anatenga mafuta odzoza, nadzoza kacisi, ndi ronse ziti m'mwemo, nazipatula.
11 Ndipo anawazako pa guwa la nsembe kasanu ndi kawiri, nadzoza guwa la nsembe, ndi zipangizo zace zonse, ndi mkhate ndi tsinde lace, kuzipatula.
12 Ndipo anatsanulirako mafuta odzoza pamutu pa Aroni, namdzoza kumpatula,
13 Ndipo Mose anatenga ana a Aroni, nawabveka maraya a m'kati, nawamanga m'cuuno ndi mipango, nawamanga akapa; monga Yehova adauza Mose.
14 Ndipo anabwera nayo ng'ombe ya nsembe yaucimo; ndipo Aroni ndi ana ace amuna anaika manja ao pa mutu wa ng'ombe ya nsembe yaucimo.
15 Ndipo anaipha; ndi Mose anatenga mwaziwo, naupaka ndi cala cace pa nyanga za guwa la nsembe pozungulira; nayeretsa guwa la nsembe, nathira mwazi patsinde pa guwa la nsembe, nalipatula, kuti alicitire colitetezera.
16 Ndipo anatenga mafuta onse a pamatumbo, ndi cokuta ca mphafa, ndi imso ziwiri, ndi mafuta ace, ndipo Mose anazitentha pa guwa la nsembe.
17 Koma ng'ombeyo, ndi cikopa cace, ndi nyama yace, ndi cipwidza cace, anazitentha ndi mote kunja kwa cigono; monga Yehova adamuuza Mose.
18 Ndipo anabwera nayo nkhosa yamphongo ya nsembe yopsereza; ndipo Aroni ndi ana ace amuna anaika manja ao pamutu pa mphongoyo.
19 Ndipo anaipha; ndi Mose anawaza mwazi wace pa guwa la nsembe pozungulira.
20 Ndipo anapadzula mphongoyo ziwalo zace; ndi Mose anatentha mutuwo ndi ziwalo, ndi mafuta.
21 Koma anatsuka matumbo ndi miyendo ndi madzi; ndi Mose anatentha mphongo yonse pa guwa la nsembe; ndiyo nsembe yopsereza yocita pfungo lokoma; ndiyo nsembe yamoto ya kwa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.
22 Ndipo anabwera nayo nkhosa yamphongo yinayo, ndiyo mphongo ya kudzaza manja; ndipo Aroni ndi ana ace amuna anaika manja ao pa mutu wa mphongoyo.
23 Ndipo anaipha; ndi Mose anatengako mwazi wace naupaka pa ndewerere ya khutu la ku dzanja lamanja la Aroni, ndi pa cala cacikuru ca ku dzanja lamanja lace, ndi pa cala cacikuru ca phazi lace la ku dzanja lamanja.
24 Pamenepo anabwera nao ana amuna a Aroni, ndi Mose anatengako mwazi, naupaka pa ndewerere ya khutu lao la ku dzanja lamanja, ndi pa cala cacikuru ca ku dzanja lamanja lao, ndi pacala cacikuru ca phazi lao la ku dzanja lamanja; ndipo Mose anawaza mwaziwo pa guwa la nsembe pozungulira,
25 Ndipo anatenga mafutawo ndi mcira wamafuta, ndi mafuta onse a pamatumbo, ndi cokuta ca mphafa, ndi imso ziwiri, ndi mafuta ace, ndi mwendo wathako wa ku dzanja lamanja;
26 ndipo mu mtanga wa mkate wopanda cotupitsa wokhala pamaso pa Yehova, anatengeramo kamtanda kamodzi kopanda cotupitsa, ndi kamtanda kamodzi ka mkate wamafuta, ndi kamtanda kamodzi kaphanthi, natiika pa mafutawo, ndi pa mwendo wathako wa ku dzanja lamanja;
27 anaika zonsezi m'manja mwa Aroni, ndi m'manja mwa ana ace amuna, naziweyula nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
28 Pamenepo Mose anazicotsa ku manja ao, nazitentha pa guwa la nsembe, pa nsembe yopsereza; ndizo nsembe zodzaza manja zocita pfungo lokoma; ndiyo nsembe yamoto ya kwa Yehova.
29 Ndipo Mose anatenga ngangayo naiweyula, nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ndilo gawo la Mose la ku nkhosa yamphongo ya kudzaza manja; monga Yehova adamuuza Mose.
30 Ndipo Mose anatengako mafuta odzoza, ndi mwazi unakhala pa guwa la nsembewo, naziwaza pa Aroni, pa zobvala zace, ndi pa ana ace amuna, ndi pa zobvala za ana ace amuna omwe; napatula Aroni, ndi zobvala zace, ndi ana ace amuna, ndi zobvala za ana ace amuna omwe.
31 Ndipo Mose anati kwa Aroni ndi kwa ana ace amuna, Phikani nyamayi pakhomo pa cihema cokomanako; ndipo muidyere komweko ndi mkate uli mu mtanga wa nsembe zodzaza manja, monga ndinauza, ndi kuti, Aroni ndi ana ace aidye.
32 Koma cotsalira ca nyama ndi mkate mucitenthe ndi moto.
33 Ndipo musaturuka pa khomo la cihema cokomanako masiku asanu ndi awiri, kufikira anakwanira masiku a kudzaza manja kwanu; pakuti adzaze manja anu masiku asanu ndi awiri.
34 Monga anacita lero lino, momwemo Yehova anauza kucita, kukucitirani cotetezera.
35 Ndipo mukhale pakhomo pa cihema cokomanako masiku asanu ndi awiri, usana ndi usiku, ndi kusunga cilangizo ca Yehova, kuti mungafe; pakuti anandiuza kotero.
36 Ndipo Aroni ndi ana ace amuna anacita zonse zimene Yehova anauza pa dzanja la Mose.
1 Ndipo kunali, tsiku lacisanu ndi citatu, kuti Mose anaitana Aroni ndi ana ace amuna, ndi akuru a Israyeli;
2 ndipo anati kwa Aroni, Dzitengere mwana wa ng'ombe wamwamuna, akhale nsembe yaucimo, ndi nkhosa yamphongo ikhale nsembe yopsereza, zopanda cirema, nubwere nazo pamaso pa Yehova.
3 Nunene kwa ana a Israyeli, ndi kuti, Dzitengereni tonde akhale nsembe yaucimo; ndi mwana wa ng'ombe, ndi mwana wa nkhosa, a caka cimodzi, opanda cirema, akhale nsembe yopsereza;
4 ndi ng'ombe, ndi nkhosa yamphongo zikhale zakuyamika, kuziphera nsembe pamaso pa Yehova; ndi nsembe yaufa yosanganiza ndi mafuta; pakuti lero Yehova wakuonekerani inu.
5 Pamenepo anatenga zimene Mose anawauza, napita nazo pakhomo pa cihema cokomanako; ndi msonkhano wonse unasendera kufupi nuimirira pamaso pa Yehova,
6 Ndipo Mose anati, Ici ndi cimene Yehova anakuuzani kuti mucicite; ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera kwa inu.
7 Ndipo Mose anati kwa Aroni, Sendera kufupi kwa guwa la nsembe, nukonze nsembe yako yaucimo, ndi nsembe yako yopsereza, nudzicitire wekha ndi anthuwo cotetetezera; nupereke coperekaca anthu, ndi kuwacitira cotetezera; monga Yehova anauza.
8 Pamenepo Aroni anasendera kufupi kwa guwa la nsembe, napha mwana wa ng'ombe wa nsembe yaucimo, ndiyo ya kwa iye yekha.
9 Ndipo ana a Aroni anasendera nao mwazi kwa iye; ndipo anabviika cala cace m'mwazimo naupaka pa nyanga za guwa la nsembe, nathira mwaziwo patsinde pa guwa la nsembe;
10 koma mafutawo, ndi imso, ndi cokuta ca mphafa za nsembe yaucimo, anazitentha pa guwa la nsembe; monga Yehova anauza Mose.
11 Ndipo anatentha ndi moto nyamayi ndi cikopa kunja kwa cigono.
12 Ndipo anapha nsembe yopsereza; ndi ana a Aroni anapereka mwaziwo kwa iye, ndipo anauwaza pa guwa la nsembe pozu ngulira.
13 Ndipo anapereka nsembe yopsereza kwa iye, ciwalo ciwalo, ndi mutu wace; ndipo anazitentha pa guwa la nsembe.
14 Ndipo anatsuka matumbo ndi miyendo, nazitentha pa nsembe yopsereza pa guwa la nsembe.
15 Ndipo anabwera naco copereka ca anthu, natenga mbuzi ya nsembe yaucimo ndiyo ya kwa anthu, naipha, naipereka nsembe yaucimo, monga yoyamba ija.
16 Ndipo anabwera nayo nsembe yopsereza naipereka monga mwa lemba lace.
17 Ndipo anabwera nayo nsembe yaufa, natengako wodzala dzanja, nautentha pa guwa la nsembe, angakhale adatentha nsembe yopsereza ya m'mawa.
18 Anaphanso ng'ombe, ndi nkhosa yamphongoyo, ndizo nsembe zoyamika za anthu; ndi ana a Aroni anapereka kwa iye mwaziwo, ndipo anauwaza pa guwa la nsembe pozungulira, ndi mafuta a ng'ombe;
19 ndi a nkhosa, ndi mcira wamafuta, ndi cophimba matumbo, ndi imso, ndi cokuta ca mphafa;
20 ndipo anaika mafuta pa ngangazo, natentha mafutawo pa guwa la nsembe.
21 Ndipo Aroni anaweyula ngangazo ndi mwendo wathako wa ku dzanja lamanja zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; monga iye anauza Mose.
22 Ndipo Aroni anakweza dzanja lace kulozera anthu, nawadalitsa; natsika kuja anapereka nsembe yaucimo, ndi nsembe yopsereza, ndi nsembe zoyamika.
23 Ndipo Mose ndi Aroni analowa ku cihema cokomanako, naturuka, nadalitsa anthu; ndipo ulemero wa Yehova unaonekera kwa anthu onse.
24 Ndipo unaturuka mota pamaso ya Yehova, nunyeketsa nsembe yopsereza ndi mafuta pa guwa la nsembe; ndipo pakuciona anthu onse anapfuula, nagwa nkhope zao pansi.
1 Ndipo ana a Aroni, Nadabu ndi Abihu anatenga yense mbale yace ya zofukiza, naikamo moto, naikapo cofukiza, nabwera nao pamaso pa Yehova moto wacilendo, umene sanawauza.
2 Ndipo panaturuka moto pamaso pa Yehova, nuwatha, nafa iwo pamaso pa Yehova.
3 Ndipo Mose anati kwa Aroni, Ici ndi cimene Yehova ananena, ndi kuti, Mwa iwo akundiyandikiza ndipatulidwa Ine, ndi pamaso pa anthu onse ndilemekezedwa. Ndipo Aroni anakhala cete.
4 Ndipo Mose anaitana Misayeli ndi Elizafana, ana a Uziyeli, mbale wa atate wa Aroni, nanena nao, Senderani pafupi, nyamulani abale anu muwacotse pakhomo pa malo opatulika kumka nao kunja kwa cigono.
5 Pamenepo anasendera pafupi, nawanyamula osawabvula maraya ao a m'kati, kumka nao kunja kwa cigono, monga Mose adauza.
6 Ndipo Mose anati kwa Aroni, ndi kwa Eleazara ndi ltamara ana ace, Musawinda tsitsi, musang'amba zobvala zanu; kuti mungafe, ndi kuti angakwiye iye ndi khamu lonse; koma abale anu, mbumba yonse ya Israyeli, alire cifukwa ca motowu Yehova anauyatsa.
7 Ndipo musaturuka pakhomo pa cihema cokomanako, kuti mungafe, pakuti mafuta odzoza a Yehova ali pa inu. Ndipo anacita monga mwa mau a Mose.
8 Ndipo Yehova ananena ndi Aroni, nati,
9 Usamamwa vinyo, kapena coledzeretsa, iwe ndi ana ako omwe, m'mene mulowa m'cihema cokomanako, kuti mungafe; likhale lemba losatha mwa mibadwo yanu;
10 ndi kuti musiyanitse pakati pa copatulika ndi cosapatulika, ndi pakati pa codetsa ndi coyera;
11 ndi kuti muphunzitse ana a Israyeli malemba onse amene Yehova analankhula nao ndi dzanja la Mose.
12 Ndipo Mose ananena ndi Aroni, ndi Eleazara ndi Itamara, ana ace otsala, Tengani nsembe yaufa yotsalira ku nsembe zamoto za Yehova, ndi kuidya yopanda cotupitsa pafupi pa guwa la nsembe; pakuti ndiyo yopatulikitsa;
13 ndipo muziidyera kumalo kopatulika, popeza ndiyo gawo lako, ndi gawo la ana ako, locokera ku nsembe zamoto za Yehova; pakuti anandiuza cotero.
14 Ndi nganga yoweyula ndi mwendo wokweza mudyere izi pamalo poyera; iwe ndi ana ako amuna, ndi ana ako akazi omwe, popeza zapatsidwa gawo lako ndi gawo la ana ako amuna, zocokera ku nsembe zoyamika za ana a Israyeli.
15 Mwendo wokweza, ndi nganga yoweyula adze nazo pamodzi ndi nsembe zamoto zamafuta, aziweyule nsembe yoweyula pamaso pa Yehova; ndipo zikhale zako ndi za ana ako amuna, mwa lemba losatha; monga Yehova anauza.
16 Ndipo Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yaucimo, ndipo, taonani, adaitentha.
17 Ndipo anapsa mtima pa Eleazara ndi Itamara, ana otsalawo a Aroni, nati, Mwalekeranji kudya nsembe yaucimo m'malo opatulika, pakuti ndiyo yopatulikitsa, ndipo iye anakupatsani iyo, kucotsera nayo mphulupulu ya khamulo, kuwacitira cowatetezera pamaso pa Yehova?
18 Taonani, sanalowa nao mwazi wace m'malo opatulika m'katimo; mukadaidyera ndithu m'malo opatulika, monga ndinakuuzani.
19 Ndipo Aroni analankhula ndi Mose, nati, Taonani, lero abwera nayo nsembe yao yaucimo ndi nsembe yao yopsereza pamaso pa Yehova; ndipo zandigwera zotere; ndikadadya nsembe yaucimo lero, kukadakomera kodi pamaso pa Yehova?
20 Pamene Mose adamva ici cidamkomera pamaso pace.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati nao,
2 Nenani ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Izi ndi zamoyo zimene muyenera kumadya mwa nyama zonse ziri pa dziko lapansi.
3 Nyama iri yonse yogawanika ciboda, nikhala yogawanikadi ciboda, ndi yobzikula, imeneyo muyenera kudya.
4 Koma izi zokha simuyenera kuzidya mwa zobzikulazo, kapena zogawanika ciboda; ngamila, angakhale abzikula, koma yosagawanika ciboda, muziiyesa yodetsedwa.
5 Ndi mbira, ingakhale ibzikula koma yosagawanika ciboda, muiyese yodetsedwa.
6 Ndi kalulu, popeza abzikula koma wosagawanika ciboda, mumuyese wodetsedwa.
7 Ndi nkhumba, popeza igawanika ciboda, nikhala yogawanikadi ciboda, koma yosabzikula, muiyese yodetsedwa.
8 Nyama yace musamaidya, mitembo yace musamaikhudza; muziyese zodetsedwa.
9 Mwa zonse ziri m'madzi muyenera kumadya izi: ziri zonse ziti nazo zipsepse ndi mamba m'madzi, m'nyanja, ndi m'mitsinje, zimenezo muyenera kumadya.
10 Koma ziti zonse ziribe zipsepse ndi mamba m'nyanja, ndi m'mitsinje, mwa zonse zokwawa za m'madzi, ndi mwa zamoyo zonse ziri m'madzi, muziziyesa zonyansa;
11 inde muziyese zonyansa; musamadya nyama zao; mitembo yao zikunyansireni.
12 Ziri zonse zopanda zipsepse kapena mamba m'madzimo muziyese zonyansa.
13 Ndipo mwa mbalame muziziyesa zonyansa izi; siziyenera kuzidya, zonyansa ndi izi: mphungu, ndi nkhwazi, ndi cikambi;
14 ndi muimba, ndi mphamba mwa mtundu wace;
15 kungubwi mwa mtundu wace;
16 ndi nthiwatiwa, ndi cipudo, ndi kakoa, ndi kabawi mwa mtundu wace;
17 ndi nkhutunkhutu ndi nswankhono ndi mancici;
18 tsekwe, bvuwo, ndi dembu;
19 indwa, ndi cimeza monga mwa mtundu wace, ndi sadzu, ndi mleme.
20 Zokwawa zonse zakuuluka zokhala ndi miyendo inai, muziyesa izi zonyansa,
21 Koma muyenera kudya izi mwa zokwawa zonse zakuuluka, zokhala ndi miyendo inai, zokhala ndi miyendo pa mapazi ao, ya kuthumpha nayo pansi; mwa zimenezi muyenera kudya izi:
22 dzombe mwa mtundu wace, ndi cirimamine mwa mitundu yace, ndi njenjete mwa mtundu wace ndi tsokonombwe mwa mitundu yace.
23 Koma zokwawa zonse zakuuluka, za miyendo inai, muziyese zonyansa.
24 Ndipo izi zikudetsani: ali yense akhudza mtembo wace adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo;
25 ndipo ali yense akanyamulako nyama ya mtembo wace azitsuka zobvala zace, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
26 Nyama iri yonse yakugawanika ciboda, koma yosagawanikitsa, ndi yosabzikula, muiyese yodetsa; ali yense wakuikhudza adzakhala wodetsedwa.
27 Ndipo iri yonse iyenda yopanda ciboda mwa zamoyo zonse za miyendo inai, muiyese yodetsedwa; ali yense wokhudza mtembo wace adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
28 Ndipo iye amene akanyamula mtembo wace atsuke zobvala zace, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo; muziyese izi zodetsa.
29 Ndipo izi ndi zimene muziziyesa zodetsedwa mwa zinthu zokwawa zakukwawa pansi; likongwe, ndi mbewa, ndi msambulu mwa mtundu wace;
30 ndi gondwa, ndi mng'anzi, ndi buluzi, ndi dududu, ndi mfuko.
31 Izi ndi zimene muziyese zodetsa, mwa zonse zakukwawa; ali yense azikhudza zitafa, adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
32 Ndipo ciri conse cakufa ca izi cikagwera kanthu, kanthuka kadzakhala kodetsedwa; ngakhale cipangizo camtengo, kapena cobvala, kapena cikopa kapena thumba, cipangizo ciri conse cimene agwira naco nchito, acibviike m'madzi, ndipo cidzakhala codetsedwa kufikira madzulo; pamenepo cidzakhala coyera.
33 Ndipo ciri conse ca izi cikagwa m'cotengera ciri conse cadothi, cinthu cokhala m'mwemo cidetsedwa, ndi cotengeraco muciswe.
34 Cakudya ciri conse cokhala m'mwemo, cokonzeka ndi madzi, cidzakhala codetsedwa; ndi cakumwa ciri conse m'cotengera cotere cidzakhala codetsedwa.
35 Ndipo kanthu ka mtembo wace kakagwa pa zinthu ziri zonse zidzakhala zodetsedwa; ngakhale mcembo kapena mphika wobvundikika, aziswe; zodetsa izi, muziyese zodetsedwa.
36 Koma kasupe kapena citsime muli madzi, zidzakhala zoyera; koma iye amene akhudza mitembo yao adzadetsedwa.
37 Ndipo kanthu ka mtembo wace kakagwa pa mbeu yofesa, ikati ifesedwe, idzakhala yoyera.
38 Koma akathira madzi pa mbeuyi, ndi kanthu ka mtembo wace kakagwapo, muiyese yodetsedwa.
39 Ndipo ikafa nyama yakudya, iye amene akhudza mtembo wace adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
40 Ndipo iye wakudya kanthu ka mtembo wace azitsuka zobvala zace, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo; iyenso wakunyamula mtembo wace atsuke zobvala zace, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
41 Ndipozokwawazonsezakukwawa pa dziko lapansi zikhale zonyansa; musamazidya.
42 Zonse zoyenda cafufumimba, ndi zonse za miyendo inai, kapena zonse zokhala nayo miyendo yambiri ndi zokwawa zonse zakukwawa pansi, musamazidya; popeza ndizo zonyansa.
43 Musamadzinyansitsa ndi cokwawa ciri conse cakukwawa, musamadzidetsa nazo, kuti mukadziipse nazo.
44 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu; potero dzipatuleni, ndipo muzikhala oyera; pakuti Ine ndine woyera; ndipo musamadziipsa ndi cokwawa ciri conse cakukwawa pansi.
45 Pakuti Ine ndine Yehova amene ndinakukwezani kukuturutsani m'dziko la Aigupto, ndikhale Mulungu wanu; cifukwa cace mukhale oyera, popeza ine ndine woyera.
46 Ici ndi cilamulo ca nyama, ndi ca mbalame, ndi ca zamoyo zonse zakuyenda m'madzi, ndi ca zamoyo zonse zakukwawa pansi;
47 kusiyanitsa pakati zodetsa ndi zoyera, ndi pakati pa zamoyo zakudya ndi zamoyo zosadya.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2 Nena ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Akaima mkazi, nakabala mwana wamwamuna, adzakhala wodetsedwa masiku asanu ndi awiri; monga masiku ace akukhala padera, podwala iye, adzakhalawodetsedwa.
3 Ndipo tsiku lacisanu ndi citatu adule khungu la mwanayo.
4 Ndipo akhale m'mwazi wa kumyeretsa kwace masiku makumi atatu kudza atatu; asakhudze kanthu kopatulika, kapena kulowa m'malo opatulika, kufikira adakwanira masiku a kumyeretsa kwace.
5 Koma akabala mwana wamkazi, akhale wodetsedwa masabata awiri, monga umo amakhala padera; ndipo adzakhala m'mwazi wa kumyeretsa kwace masiku makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi limodzi.
6 Ndipo atakwanira masiku a kumyeretsa kwace pa mwana wamwamuna, kapena mwana wamkazi, adze naye mwana wa nkhosa wa caka cimodzi ikhale nsembe yopsereza, ndi bunda, kapena njiwa zikhale nsembe yaucimo, ku khomo la cihema cokomanako, kwa wansembe;
7 ndipo iye abwere nayo pamaso pa Yehova, namcitire comtetezera mkaziyo, ndipo adzakhala woyeretsedwa wocira kukha mwazi kwace.
8 Ici ndi cilamulo ca kwa iye wakubala, kapena mwana wamwamuna kapena wamkazi. Ndipo cuma cace cikapanda kufikira nkhosa, atenge njiwa ziwiri kapena maunda awiri; lina likhale nsembe yopsereza, ndi lina nsembe yaucimo; ndi wansembe amcitire comtetezera, ndipo adzakhalawoyera.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,
2 Ngati munthu ali naco cotupa, kapena nkhanambo, kapena cikanga pa khungu la thupi lace, ndipo isandulika nthenda yakhate pa khungu la thupi lace, azifika kwa Aroni wansembe, kapena kwa mmodzi wa ana ace ansembe;
3 ndipo wansembe aione nthenda pa khungu la thupi; ndipo ngati tsitsi la panthenda lasanduka la mbu, ndi nthenda ikaoneka yapitirira khungu la thupi lace, ndiyo nthenda yakhate; ndipo wansembe amuone, namuche wodetsedwa.
4 Koma ngati cikanga cikhala cotuwa pa khungu la thupi lace, ndipo cikaoneka cosapitirira khungu, ndi tsitsi lace losasanduka loyera, pamenepo wansembe ambindikiritse wanthendayo masiku asanu ndi awiri;
5 ndipo wansembe amuonenso tsiku lacisanu ndi ciwiri; ndipo taonani, monga momwe apenyera iye, nthenda yaima, nthenda siinapitirira pakhungu, pamenepo wansembe ambindikiritsenso masiku asanu ndi awiri ena;
6 ndipo wansembe amuonenso tsikulacisanu ndi ciwiri, ndipo taonani, nthenda yazimba yosapitirira khungu nthendayi, pamenepo wansembe amuche iye woyera, ndiyo nkhanambo cabe; ndipo atsuke zobvala zace, ndiye woyera;
7 koma nkhanambo ikapitirira khungu, atadzionetsakwa wansembe kuti achedwe woyera, adzionetsenso kwa wansembe;
8 ndipo wansembe aone, ndipo taonani, ngati nkhanambo yapitirira khungu, wansembe amuche wodetsedwa, ndilo khate.
9 Pamene nthenda yakhate iri mwa munthu, azimfikitsa kwa wansembe;
10 ndipo wansembe aone, ndipo taonani, ngati pali cotupa coyera pakhungu, ndipo casanduliza tsitsi likhale loyera, ndipo pacotupa pali mnofu wofiira,
11 ndilo khate lakale pa khungu la thupi lace, ndipo wansembe amuche wodetsedwa; asambindikiritse popeza ali wodetsedwa.
12 Ndipo ngati khate libukabuka pakhungu, ndi khate lakuta khungu lonse la wanthendayo kuyambira mutu wace kufikira mapazi ace, monga momwe apenyera wansembe;
13 pamenepo wansembe aone, ndipo taonani, ngati khate lakuta thupi lace, amuche woyera wanthendayo; patuwa ponsepo; ndiye woyera.
14 Koma tsiku liri lonse ukaoneka pa iye mnofu wofiira, adzakhala wodetsedwa,
15 Ndipo wansembe aone mnofu wofiirawo, namuche wodetsedwa; mnofu wofiira ndiwo wodetsa; ndilo khate.
16 Kapena mnofu wofiira ukasandukanso, nusandulika wotuwa, afike kwa wansembe,
17 ndi wansembe amuone, ndipo taonani, ngati nthenda yasandulika yotuwa, wansembe amuche woyera wanthendayo; ndiye woyera.
18 Ndipo pamene thupi liri ndi cironda pakhungu pace, ndipo capola,
19 ndipo padali cironda pali cotupa coyera, kapena cikanga cotuuluka, pamenepo acionetse kwa wansembe; ndipo wansembe aone,
20 ndipo taonani, ngati cioneka cakumba kubzola khungu, ndipo tsitsi lace lisanduka lotuwa, pamenepo wansembe amuche wodetsedwa; ndiyo nthenda yakhate yabuka m'cirondamo.
21 Koma wansembe akaciona, ndipo taonani, palibe tsitsi loyera pamenepo, ndipo sicinakumba kubzola khungu, koma cazimba, pamenepo wansembe ambindikiritse masiku asanu ndi awiri;
22 ndipo ngati capitirira khungu, wansembe amuche wodetsedwa; ndilo khate.
23 Koma ngati cikanga caima pomwepo, cosakula, ndico cipsera ca cironda; ndipo wansembe amuche woyera.
24 Kapena pamene thupi lidapsya ndi mota pakhungu pace, ndipo mnofu wofiira wakupsyawo usanduka cikanga cotuuluka, kapena cotuwa:
25 pamenepo wansembe acione; ndipo taonani, ngati tsitsi la cikanga lasanduka lotuwa, ndipo cioneka cakumba kubzola khungu; pamenepo ndilo khate lobuka m'kupsyamo; ndipo wansembe azimucha wodetsedwa ndi nthenda yakhate.
26 Koma akaonapo wansembe, ndipo taonani, mulibe tsitsi loyera m'cikangamo, ndipo sicikumba kubzola khungu, koma cazimba; pamenepo wansembe ambindikiritse masiku asanu ndi awiri;
27 ndipo wansembe amuone tsiku lacisanu ndi ciwiri; ngati cakula pakhungu, wansembe amuche wodetsedwa; ndiyo nthenda yakhate,
28 Ndipo ngati cikanga ciima pomwepo, cosakula pakhungu koma cazimba; ndico cotupa ca kupsya; ndipo wansembe amuche woyera; pakuti ndico cipsera ca kupsya.
29 Ndipo ngati mwamuna kapena mkazi ali ndi nthenda pamutu kapena pandebvu,
30 wansembe aziona nthenda; ndipo taonani, ngati ioneka yokumba kubzola khungu, ndipo pali tsitsi loyezuka lotetemera; pamenepo wansembe amuche wodetsedwa; ndiyo mfundu, ndilo khate la mutu kapena ndebvu.
31 Ndipo wansembe akaona nthenda yamfundu, ndipo taonani, ioneka yosakumba kubzola khungu, ndipo palibe tsitsi lakuda pamenepo, wansembe ambindikiritse iye ali ndi mfundu masiku asanu ndi awiri;
32 ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri wansembe aone nthendayi; ndipo taonani, ngati mfundu njosakula, ndipo mulibe tsitsi loyezuka, ndipo mfundu ikaoneka yosakumba kubzola khungu,
33 pamenepo azimeta, koma osameta pamfundu; ndipo wansembe ambindikiritse iye wamfundu masiku asanu ndi awiri ena;
34 ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri aone mfunduyo; ndipo taonani, ngati mfundu njosakula pakhungu, ndipo ioneka yosakula kubzola khungu, wansembe amuche woyera, ndipo iye atsuke zobvala zace, nakhala woyera.
35 Koma ngati mfundu ikula pakhungu atachedwa woyera;
36 pamenepo wansembe amuone, ndipo taonani, ngati mfundu yakula pakhungu, wansembe asafunefune tsitsi loyezuka, ndiye wodetsedwa.
37 Koma monga momwe apenyera iye, ngati mfundu yaima pomwe, ndipo pamera tsitsi lakuda, mfundu yapola, ndiye woyera, ndipo wansembe amuche woyera.
38 Ndipo ngati mwamuna kapena mkazi ali ndi zikanga pa khungu la thupi lace, zikanga zoyerayera;
39 wansembe aziona; ndipo taonani ngati zikanga ziri pa khungu la thupi lao zikhala zotuwatuwa; ndilo thuza labuka pakhungu; ndiye woyera.
40 Ndipo ngati tsitsi la munthu lathothoka, ndiye wadazi; koma woyera.
41 Ndipo ngati tsitsi lathothoka pamphumi pace ndiye wa masweswe, koma woyera.
42 Koma ngati pali nthenda yotuuluka pakati pa dazi lace la pamutu, kapena la pamphumi, ndipo khate lirikubuka pakati pa dazi lace la pamutu, kapena la pamphumi.
43 Pamenepo wansembe azimuona, ndipo taonani, ngati cotupa cace ca nthenda ciri cotuuluka pa dazi la pa mutu wace, kapena la pamphumi pace, monga maonekedwe a khate pa khungu la thupi;
44 ndiye wakhate, ndiye wodetsedwa; wansembe amuchetu wodetsedwa; nthenda yace iri pamutu pace.
45 Ndipo azing'amba zobvala zace za wakhate ali ndi nthendayo, ndi tsitsi la pamutu pace lizikhala lomasuka, naphimbe iye mlomo wace wa m'mwamba, napfuule, Wodetsedwa, wodetsedwa!
46 Masiku onse nthenda ikali pa iye azikhala wodetsedwa; ali wodetsedwa, agone pa yekha pokhala pace pakhale kunja kwa cigono.
47 Ndiponso ngati nthenda yakhate iri pa cobvala caubweya, kapena cathonje;
48 ngakhale iri pamuyaro, kapena pamtsendero, cathonje, kapena caubweya, ngakhale iri pa cikopa, kapena pa cinthu ciri conse copanga ndi cikopa;
49 ngati nthenda iri yobiriwira, kapena yofiira pacobvala, kapena pacikopa, kapena pamuyaro, kapena pamtsendero, kapena pa cinthu ciri conse copangika ndi cikopa, ndiyo nthenda yakhate; aziionetsa kwa wansembe;
50 ndipo wansembe aone nthendayo, nabindikiritse ciija ca nthenda masiku asanu ndi awiri;
51 naone nthenda tsiku lacisanu ndi ciwiri; ngati nthenda yakula pacobvala, ngakhale pamuyaro, kapena pamtsendero, kapena pacikopa, ziri zonse zanchito zopangika ndi cikopa; nthendayo ndiyo khate lofukuta; ndico codetsedwa.
52 Ndipo atenthe cobvalaco ngakhale muyaro wace, ngakhale mtsendero wace, caubweya kapena cathonje, kapena ciri conse cacikopa ciri ndi khate, ndilo khate lofetsa; acitenrhe ndi mote.
53 Ndipo wansembe akaona, ndipo taonani, nthenda njosakula pacobvala, kapena pamuyaro, kapena pamtsendero, kapena pa cinthu ciri conse copangika ndi cikopa;
54 pamenepo wansembe aziuza kuti atsuke cija pali khate, nacibindikiritse masiku asanu ndi awiri ena;
55 ndipo wansembe aone nthenda ataitsuka, ndipo taonani, ngati nthendayi siinasandulika maonekedwe ace, yosakulanso nthenda, ndico codetsedwa; ucitenthe ndi moto; ndilo pfunka, kungakhale kuyera kwace kuli patsogolo kapena kumbuyo.
56 Ndipo wansembe akaona, ndipo taonani, nthenda yazimba ataitsuka, pamenepo aikadzule pa cobvala, kapena cikopa, kapena muyaro, kapena mtsendero;
57 ndipo ikaonekabe pacobvala, ngakhale pamuyaro, kapena pamtsendero, kapena pa cinthu ciri conse copangika ndi cikopa, irikubukanso; ucitenthe ndi moto cija canthenda.
58 Ndipo ukatsuka cobvalaco, kapena muyaro, kapena mtsendero, kapena cinthu ciri conse copangika ndi cikopa, ngati nthenda yalekapo pa cimeneco, acitsukenso kawiri, pamenepo ciri coyera.
59 Ici ndi cilamulo ca nthenda yakhate iri pa cobvala caubweya kapena cathonje, ngakhale pamuyare, kapena pamtsendero, kapena pa cinthu ciri conse copangika ndi cikopa; kucicha coyera kapena kucicha codetsa.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose nati,
2 Cilamulo ca wakhate tsiku la kumyeretsa kwace ndi ici: azidza naye kwa wansembe;
3 ndipo wansembe aturuke kumka kunja kwa cigono; ndipo wansembe aone, ndipo taonani, ngati nthenda Yakhate yapola pa wakhateyo;
4 pamenepo wansembe auze kuti amtengere iye wakuti akonzedwe, mbalame ziwiri zoyera zamoyo, ndi mtengo wamkungudza, ndi, ubweya wofiira, ndi hisope;
5 ndipo wansembe auze kuti aphe mbalame imodzi m'mbale yadothi pamwamba pa madzi oyenda;
6 natenge nbalame yamoyo, ndi mtengo wankungudza, ndi ubweya wofiira, ndi hisope, nazibviike pamodzi ndi mbalame yamoyo m'mwazi wa mbalame adaipha pamwamba pa madzi oyenda;
7 nawaze kasanu ndi kawiri iye amene akuti amyeretse khate lace, namuche woyera, nataye mbalame yamoyo padambo poyera.
8 Ndipo iye wakutiayeretsedwe atsuke zobvala zace, namete tsitsi lace lonse, nasambe madzi, nakhale woyera; ndipo atatero alowe kucigono, koma agone pa bwalo la hema wace masiku asanu ndi awiri.
9 Ndipo tsiku lacisanu ndi ciwiri kudzakhala kuti amete tsitsi lace lonse la pamutu pace, ndi ndebvu zace, ndi nsidze zace, inde amete tsitsi lace lonse; natsuke zobvala zace, nasambe thupi lace ndi madzi, nakhale woyera.
10 Ndipo tsiku lacisanu ndi citatu atenge ana a nkhosa awiri, amuna opanda cirema, ndi mwana wa nkhosa mmodzi wamkazi wa caka cimodzi wopanda cirema, ndi atatu a magawo khumi a ufa wosalala ukhale nsembe yaufa, wosanganiza ndi mafuta, ndi muyeso umodzi wa mafuta.
11 Ndipo wansembe amene amyeretsayo, amuike munthu uja wakuti ayeretsedwe, ndi zinthu zija, pamaso pa Yehova, pa khomo la cihema cokomanako;
12 ndipo wansembe atenge mwana wa nkhosa mmodzi wamwamuna, nabwere naye akhale nsembe yoparamula, pamodzi ndi muyeso uja wa mafuta, naziweyule nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
13 Ndipo akaphere mwana wa nkhosa wamwamuna paja amapherapo nsembe yaucimo, ndi nsembe yopsereza, pa malo popatulika; pakuti monga nsembe yaucimo momwemo nsembe yoparamula, nja wansembe; ndiyo yopatulikitsa.
14 Ndipo wansembe atengeko mwazi wa nsembe yoparamula, ndipo wansembe aupake pa ndewerere ya khutu la ku dzanja lamanja la iye wakuti ayeretsedwe, ndi pa cala cacikuru ca dzanja lace lamanja, ndi pa cala cacikuru ca phazi lace la ku dzanja lamanja;
15 ndipo wansembe atengeko muyeso wa mafuta, nawathire pa cikhato ca dzanja lace lamanzere la iye mwini;
16 ndipo wansembe abviike cala cace ca dzanja lace lamanja ca iye mwini m'mafuta ali m'dzanja lace lamanzere, nawaze mafuta kasanu ndi kawiri ndi cala cace pamaso pa Yehova;
17 ndipo wansembe apakeko mafuta okh a ria m'dzanja lace pa ndewerere ya khutu la ku dzanja lamanja la iye wakuti ayeretsedwe, ndi pa cala cacikuru ca dzanja lace lamanja, ndi pa cala cacikuru ca phazi lace la ku dzanja lamanja, pa mwazi wa nsembe yoparamula;
18 natsitsitize mafuta otsala m'dzanja lace la wansembe, pamutu pa iye wakuti ayeretsedwe; ndipo wansembe amcitire comtetezers pamaso pa Yehova.
19 Ndipo wansembe apereke nsembe yaucimo, namcitire comtetezera amene akuti ayeretsedwe, cifukwa ca kudetsedwa kwace; ndipo atatero aphe nsembe yopsereza;
20 ndipo wansembe atenthe nsembe yopsereza, ndi nsembe yaufa pa guwa la nsembe; ndipo wansembe amcitire comtetezera, ndipo adzakhala iye woyera.
21 Ndipo akakhala waumphawi cosafikana cuma cace azitenga mwana wa nkhosa mmodzi wamwamuna akhale nsembe yoparamula, aiweyule kumcitira comtetezera, ndi limodzi la magawo khumi la efa la ufa wosalala, wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa, ndi muyeso umodzi wa mafuta;
22 ndi njiwa ziwiri, kapena maunda awiri, monga akhoza kufikana; limodzi likhale la nsembe yaucimo, ndi linzace la nsembe yopsereza.
23 Ndipo tsiku lacisanu ndi citatu abwere nao kwa wansembe, ku khomo la cihema cokomanako, pamaso pa Yehova.
24 Ndipo wansembe atenge mwana wa nkhosa wa nsembe yoparamula, ndi muyeso wa mafuta, ndipo wansembe aziweyule nsembe yoweyula pamaso pa Yehova;
25 naphe mwana wa nkhosa wa nsembe yoparamula, ndipo wansembe atengeko mwazi wa nsembe yoparamula, naupake pa ndewerere ya khutu la ku dzanja lamanja la iye akuti ayeretsedwe, ndi pa cala cacikuru ca dzanja lace lamanja, ndi pa cala cacikuru ca phazi lace la ku dzanja lamanja;
26 ndipo wansembe athireko mafuta aja m'cikhato cace camanzere ca iye mwini;
27 ndipo wansembe awazeko mafuta aja ali m'dzanja lace lamanzere ndi cala cace ca dzanja lamanja, kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova;
28 ndipo wansembe apakeko mafuta aja ali m'dzanja lace pa ndewerere ya khutu la ku dzanja lamanja la iye wakuti ayeretsedwe, ndi pa cala cacikuru ca: dzanja lace lamanja, ndi pa cala cacikuru ca phazi lace la ku dzanja lamanja, pa malo paja pali mwazi wa usembe yoparamula;
29 ndipo mafuta otsala m'dzanja la wansembe atsitsitize pa mutu wa iye wakuti ayeretsedwe, kumcitira comtetezera pamaso pa Yehova.
30 Ndipo iye apereke imodzi ya njiwazo, kapena limodzi la maunda, monga akhoza kufikana nazo, limodzi la nsembe yaucimo, ndi tina la nsembe yopsereza, pamodzi ndi nsembe yaufa;
31 ndipo wansembe amcitire comtetezera pamaso pa Yehova.
32 Ici ndi cilamulo ca iye ali ndi nthenda yakhate, wosakhoza kufikana nazo zofunika pomyeretsa pace.
33 Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,
34 Mutakafika m'dziko la Kanani, limene ndikupatsani likhale lanu lanu, ndipo ndikaika nthenda yakhate m'nyumba ya dziko lanu lanu;
35 pamenepo mwini nyumbayo adzauze wansembe, kuti, Ndiyesa muli ngati nthenda m'nyumba.
36 Ndipo wansembe aziuza kuti aturutse zonse za m'nyumba, asanalowe kudzaona nthendayi, zinthu zonse ziri m'nyumba zingakhale zodetsedwa; ndipo atatero wansembe alowe kukaona nyumbayi;
37 naone nthendayo, ndipo taonani, nthenda ikakhala yosumbudzuka m'makoma a nyumba yobiriwira kapena yofiira, ndipo maonekedwe ace yakumba kubzola khoma;
38 pamenepo wansembe azituruka ku khomo la nyumba, natseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri;
39 ndipo wansembe abwerenso tsiku lacisanu ndi ciwiri, naonenso, ndipo taonani, ngati nthenda yakula m'makoma a nyumba;
40 pamenepo wansembe auze kuti agumule miyalayi pali nthenda, naitayire ku malo akuda kunja kwa mudzi;
41 napalitse nyumba m'kati monsemo, natayire ku malo akuda kunja kwa mudzi dothi adapalako;
42 natenge miyala yina, naikhazike m'male mwa miyala ija; natenge dothi tina, namatenso nyumbayo.
43 Ndipo ikabweranso nthenda, nibukanso m'nyumba atagumula miyala, ndipo atapala m'nyumba namatanso;
44 pamenepo wansembe alowe naonemo, ndipo taonani, ngati nthenda yakula m'nyumba, ndiyo khate lonyeka m'nyumba; ndiyo yodetsedwa.
45 Ndipo apasule nyumbayo, miyala yace, ndi mitengo yace, ndi dothi lace lonse kumudzi kuzitaya ku malo akuda.
46 Ndiponso iye wakulowa m'nyumba masiku ace iriyotsekedwa, adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
47 Ndipo iye wakugona m'nyumbayo atsuke zobvala zace; ndi iye wakudya m'nyumbayo atsuke zobvala zace.
48 Ndipo wansembe akalowa, nakaona, ndipo taonani, nthenda siinakula m'nyumba, ataimata nyumba; wansembe aiche nyumbayo yoyera, popeza nthenda yaleka.
49 Pamenepo atenge mbalame ziwiri, ndi mtengo wamkungudza, ndi ubweya wofiira, ndi hisope, kuti ayeretse nazo nyumbayo;
50 naphe mbalame imodzi m'mbale yadothi, pamwamba pa madzi oyenda;
51 natenge mtengo wamkungudza ndi hisope, ndi ubweya wofiira, ndi mbalame yamoyo, nazibviike m'mwazi wa mbalame yakuphayo, ndi m'madzi oyenda, nawaze kasanu ndi kawiri m'nyumba;
52 nayeretsenyumbandi mwazi wa mbalame, ndi madzi oyenda, ndi mbalame yamoyo, ndi mtengo wamkungudza, ndi hisope, ndi ubweya wofiira.
53 Koma ataye mbalame yamoyo kunja kwa mudzi kuthengo koyera; motero aicitire coitetezera nyumbayo; ndipo idzakhala yoyera.
54 Ici ndi cilamulo ca nthenda iri yonse yakhate, ndi yamfundu;
55 ndi ya khate la cobvala, ndi la nyumba;
56 ndi yacotupa, ndi yankhanambo, ndi yacikanga;
57 kulangiza tsiku loti cikhala codetsa, ndi tsiku loti cikhala coyera; ici ndi cilamulo ca khate.
1 Mose ndi Aroni, nati,
2 Nenani nao ana a Israyeli, nimuti nao, Pamene mwamuna ali yense ali ndi nthenda yakukha m'thupi mwace, akhale wodetsedwa, cifukwaca kukha kwace.
3 Ndipo kudetsedwa kwa kukha kwace ndiko: ngakhale cakukhaco cituruka m'thupi mwace, ngakhale caleka m'thupi mwace, ndiko kumdetsa kwace.
4 Kama ali yense agonapo wakukhayo ali wodetsedwa; ndi cinthu ciri conse acikhalira ciri codetsedwa.
5 Ndipo munthu ali yense wakukhudza kama wace azitsuka zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo,
6 Ndipo iye wakukhalira cinthu ciri conse adacikhalira wakukhayo atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
7 Ndipo iye wakukhudza thupi la uyo wakukhayo atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
8 Ndipo wakukhayo akalabvulira wina woyera; pamenepo atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
9 Ndipo mbereko iri yonse akwerapo wakukhayo iri yodetsedwa.
10 Ndipo munthu ali yense akakhudza kanthu kali konse kadali pansi pace adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo; ndipo iye wakunyamula zimenezo atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
11 Ndipo munthu ali yense wakukhayo akamkhudza, osasambatu m'manja m'madzi, atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
12 Ndipo zotengera zadothi wazikhudza wakukhayo, aziphwanye; ndi zamtengo, azitsuke ndi madzi.
13 Ndipo wakukhayo atayeretsedwa ku kukha kwace, adziwerengere masiku asanu ndi awiri akhale a kuyeretsa kwace, natsuke zobvala zace; nasambe thupi lace ndi madzi oyenda, nadzakhala woyera.
14 Ndipo tsiku lacisanu ndi citatu atenge njiwa ziwiri, kapena maunda awiri, nafike pamaso pa Yehova pa khomo la cihema cokomanako, nazipereke kwa wansembe;
15 ndipo wansembe azipereke izo, imodzi ikhale nsembe yaucimo, ndi yina nsembe yopsereza; ndipo wansembe amcitire comtetezera pamaso pa Yehova cifukwa ca kukha kwace.
16 Ndipo munthu ali yense akagona uipa, azisamba thupi lace lonse ndi madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
17 Ndipo cobvala ciri conse, ndi cikopa ciri conse, anagona uipa pamenepo azitsuke ndi madzi, nizidzakhala zodetsedwa kufikira madzulo.
18 Mkazi yemwe, mwamuna atagona naye, onse awiri asambe ndi madzi, nadzakhala odetsedwa kufikira madzulo.
19 Ndipo ngati mkazi ali ndi nthenda yakukha, ndi kukha kwace nkwa mwazi m'thupi mwace, akhale padera masiku asanu ndi awiri; ndipo ali yense amkhudza adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
20 Ndipo cinthu ciri conse agonapo pokhala ali padera ncodetsedwa; ndi cinthu ciri conse akhalapo ncodetsa.
21 Ndipo ali yense akhudza kama wace azitsuka zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
22 Ndipo ali yense akhudza cinthu ciri conse akhalapo iye, atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
23 Ndipo cikakhala pakama, kapena pa cinthu ciri conse akhalapo iye, atacikhudza, adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
24 Ndipo ngati mwamuna ali yense agona naye, ndi kudetsa kwace kukhala pa iye, adzakhala wodetsedwa masiku asanu ndi awiri; ndipo kama ali yense agonapo ali wodetsedwa.
25 Ndipo mkazi akakhala ndi kukha mwazi masiku ambiri, osati masiku a kuoloka kwace, kapena akamakha kupitirira nthawi ya kuoloka kwace; masiku onse cirinkukha comdetsa cace, adzakhala wodetsedwa, monga masiku a kuoloka kwace.
26 Kama ali yense agonapo masiku a kukha kwace akhale ngati kama wa kuoloka kwace; ndi cinthu ciri conse akhalapo ciri codetsedwa, ngati kudetsa kwa kuoloka kwace.
27 Ndipo munthu ali yense akakhudza zimenezi adzakhala wodetsedwa, natsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.
28 Koma akayeretsedwa kukha kwace, adziwerengere masiku asanu ndi awiri, ndipo atatero adzakhala woyeretsedwa.
29 Ndipo tsiku lacisanu ndi citatu atenge njiwa ziwiri, kapena maunda awiri, nafike nazo kwa wansembe ku khomo la cihema cokomanako.
30 Ndipo wansembe apereke limodzi likhale nsembe yaucimo, ndi linalo likhale nsembe yopsereza; ndipo wansembe amcitire comtetezera pamaso pa Yehova cifukwa ca kukha kwace komdetsa.
31 Motero muzipatula ana a Israyeli kwa kudetsedwa kwao; angafe m'kudetsedwa kwao, pamene adetsa kacisi wanga ali pakati pao.
32 Ici ndi cilamulo ca wakukha, ndi ca iye wakugona uipa, kuti kumkhalitse wodetsedwa;
33 ndi ca mkazi alinkudwala ndi kudetsedwa kwace, ndi ca iye alikukha kapena mwamuna, kapena mkazi, ndi ca iye agona ndi mkazi wodetsedwa.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, atamwalira ana amuna awiri a Aroni, muja anasendera pamaso pa Yehova, namwalira;
2 ndipo Yehova anati kwa Mose, Nena ndi Aroni mbale wako, kuti asalowe nthawi zonse m'malo opatulika m'tseri mwa nsaru yocinga, pali cotetezerapo cokhala palikasa, kuti angafe; popeza ndioneka mumtambo pacotetezerapo.
3 Aroni azilowa pa bwalo la malo opatulika nazozo: ng'ombe yamphongo ikhale ya nsembe yaucimo, ndi nkhosa yamphongo ikhale ya nsembe yopsereza.
4 Abvale maraya a m'kati a bafuta wopatulika, nakhale nazo zobvala za kumiyendo pathupi pace, nadzimangire m'cuuno ndi mpango wabafuta, nabvale nduwira yabafuta; izi ndi zobvala zopatulika; potero asambe thupi lace ndi madzi, ndi kubvala izi.
5 Ndipo ku khama la ana a Israyeli atenge atonde awiri akhale a nsembe yaucimo, ndi nkhosa yamphongo imodzi ikhale ya nsembe yopsereza.
6 Ndipo Aroni abwere nayo ng'ombe ya nsembe yaucimo, ndiyo yace yace, nacite codzitetezera iye yekha, ndi mbumba yace.
7 Ndipo atenge mbuzi ziwirizo naziimike pamaso pa Yehova pakhomo pa cihema cokomanako.
8 Ndipo Aroniayesemaere pa mbuzi ziwirizo; maere amodzi kwa Yehova, ndi amodzi kwa Azazeli.
9 Ndipo Aroni abwere nayo mbuzi imene adaigwera maere a Yehova, naiyese nsembe yaucimo.
10 Koma mbuzi imene adaigwera maere a Azazeli, aiike yamoyo pamaso pa Yehova, kuti acite nayo cotetezera, kuitumiza kucipululu ikhale ya Azazeli.
11 Ndipo Aroni abwere nayo ng'ombe ya nsembe yaucimo, ndiyo yace yace, nadzitetezere iye yekha, ndi mbumba yace, ndi kupha ng'ombe ya nsembe yaucimo ndiyo yace yace;
12 natenge mbale ya zofukiza yodzala ndi makara amoto, kuwacotsa pa guwa la nsembe, pamaso pa Yehova, ndi manja ace odzala ndi cofukiza copera ca pfungo lokoma, nalowe nayo m'tseri mwa nsaru yocinga;
13 naike cofukizaco pamoto pamaso pa Yehova, kuti mtambo wa cofukiza ciphimbe cotetezerapo cokhala pamboni, kuti angafe.
14 Ndipo atengeko mwazi wa ng'ombeyo, ndi kuuwaza ndi cala cace pacotetezerapo, mbali ya kum'mawa; nawaze mwazi ndi cala cace cakuno ca cotetezerapo kasanu ndi kawiri.
15 Pamenepo aiphe mbuzi ya nsembe yaucimo, ndiyo yophera anthu, nalowe nao mwazi wace m'tseri mwa nsaru yocinga, nacite nao mwazi wace monga umo anacitira ndi mwazi wa ng'ombe, nauwaze pacotetezerapo ndi cakuno ca cotetezerapo;
16 nacitire cotetezera malo opatulika, cifukwa ca kudetsedwa kwa ana a Israyeli, ndi cifukwa ca zolakwa zao, monga mwa zocimwa zao zonse; nacitire cihema cokomanako momwemo, cakukhala nao pakati pa zodetsa zao.
17 Ndipo musakhale munthu m'cihema cokomanako pakulowa iye kucita cotetezera m'malo opatulika, kufikira aturuka, atacita cotetezera yekha, ndi mbumba yace, ndi msonkhano wonse wa Israyeli.
18 Ndipo aturukire guwa la nsembe lokhala pamaso pa Yehova ndi kulicitira cotetezera; natengeko mwazi wa ng'ombeyo, ndi mwazi wa mbuziyo, ndi kuupaka pa nyanga za guwa la nsembe pozungulira.
19 Ndipo awazepo mwazi wina ndi cala cace kasanu ndi katatu; ndi kuliyeretsa ndi kulipatula kulicotsera zodetsa za ana a Israyeli.
20 Ndipo atatha kucitira cotetezera malo opatulika, ndi cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe, abwere nayo mbuzi yamoyo;
21 ndipo Aroni aike manja ace onse awiri pamutu pa mbuzi yamoyo, ndi kubvomereza pa iyo mphulupulu zonse za ana a Israyeli, ndi zolakwa zao zonse, monga mwa zocimwa zao zonse; naike izi pamutu pa mbuziyo, ndi kuitumiza kucipululu ndi dzanja la munthu wompangiratu,
22 ndi mbuziyo isenze yokha mphulupulu zonsezo kumka nazo ku dziko la pa lokha; ndipo azitaya mbuziyo m'cipululu.
23 Pamenepo Aroni alowe m'cihema cokomanako, nabvule zobvala zabafuta zimene anazibvala polowa m'malo opatulika, nazisiye komweko.
24 Ndipo asambe thupi lace ndi madzi kumalo kopatulika, nabvale zobvala zace, naturuke, napereke nsembe yopsereza yace, ndi nsembe yopsereza ya anthu, nacite codzitetezera yekha ndi anthu.
25 Ndipo atenthe mafuta a nsembe yaucimo pa guwa la nsembe.
26 Ndipo iye amene anacotsa mbuzi ipite kwa Azazeli atsuke zobvala zace, nasambe thupi lace ndi madzi, ndipo atatero alowenso kucigono.
27 Koma ng'ombe ya nsembe yaucimo, ndi mbuzi ya nsembe yaucimo, zimene mwazi wao analowa nao kucita nao cotetezera m'malo opatulika, aturuke nazo kunja kwa cigono; natenthe ndi mota zikopa zao, ndi nyama zao, ndi cipwidza cao.
28 Ndi iye amene anazitentha atsuke zobvala zace, nasambe thupi lace ndi madzi, ndipo atatero alowenso kucigono.
29 Ndipo lizikhala kwa Inu lemba Ilosatha; mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku lakhumi la mweziwo, muzidzicepetsa, osagwira Debito konse, kapena wa m'dziko, kapena mlendo wakukhala pakati panu;
30 popeza tsikuli adzacitira inu cotetezera, kukuyeretsani; adzakuyeretsani, kukucotserani zoipa zanu zonse pamaso pa Yehova.
31 Likhale kwa inu sabata lakupumula, kuti mudzicepetse; ndilo lemba losatha.
32 Ndipo wansembe, amene anamdzoza ndi kumdzaza dzanja lace acite nchito ya nsembe m'malo mwa atate wace, acite cotetezera, atabvala zobvala zabafuta, zobvala zopatulikazo.
33 Ndipo acite cotetezera malo opatulikatu, natetezere cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe; momwemo atetezerenso ansembe, ndi anthu onse a msonkhanowo.
34 Ndipo ici cikhale kwa inu lemba losatha, kucita cotetezera ana a Israyeli, cifukwa ca zocimwa zao zonse, kamodzi caka cimodzi. Ndipo anacita monga Yehova adauza Mose.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2 Nena ndi Aroni, ndi ana ace amuna, ndi ana a Israyeli onse, nuti nao, Ici ndi cimene Yehova wauza, ndi kuti,
3 Munthu ali yense wa mbumba ya Israyeli akapha ng'ombe, kapena mwana wa nkhosa, kapena mbuzi, m'cigono, kapena akaipha kunja kwa cigono,
4 osadza nayo ku khomo la cihema cokomanako, kuti aipereke copereka ca Yehova, ku bwalo la kacisi wa Yehova; azimuyesa munthuyu wocimwira mwazi, wakhetsa mwazi; ndipo amsadze munthuyo kumcotsa pakati pa anthu a mtundu wace;
5 kotero kuti ana a Israyeli azidza nazo nsembe zao, zimene aziphera kuthengo koyera, kuti adze nazo kwa Yehova, ku khomo la cihema cokomanako, kwa wansembe, ndi kuziphera nsembe zoyamika za Yehova.
6 Ndipo wansembeyo awaze mwaziwo pa guwa la nsembe la Yehova, pa khomo la cihema cokomanako, natenthe mafuta akhale pfungo lokoma lokwera kwa Yehova.
7 Ndipo asamapheranso ziwanda nsembe zao, zimene azitsata ndi cigololo. Ili liwakhalire lemba losatha mwa mibadwo yao.
8 Ndipo uzinena nao, Munthu ali yense wa mbumba ya Israyeli, kapena mlendo wakugonera pakati panu, amene apereka nsembe yopsereza kapena nsembe yophera,
9 osadza nayo ku khomo la cihema cokomanako, kuiphera Yehova; amsadze munthuyu kumcotsa kwa anthu a mtundu wace.
10 Ndipo munthu ali yense wa mbumba ya Israyeli, kapena mlendo wogonera pakati panu, wakudya mwazi uli wonse; nkhope yanga idzatsutsana naye munthu wakudya mwaziyo, ndi kumsadza kumcotsa kwa anthu a mtundu wace.
11 Pakuti moyo wa nyama ukhala m'mwazi; ndipo ndakupatsani uwu pa guwa la nsembe, ucite cotetezera moyo wanu; pakuti wocita cotetezera ndiwo mwazi, cifukwa ca moyo wace.
12 Cifukwa cace ndinanena kwa ana a Israyeli, Asamadya mwazi mmodzi yense wa inu, kapena mlendo ali yense wakugoneramwa inu asamadya mwazi.
13 Ndipo munthu ali yense wa ana a Israyeli, kapena mlendo wakugonera pakati pa inu, akasaka nyama kapena mbalame yakudya, nakaigwira; azikhetsa mwazi wace naufotsere ndi dothi.
14 Pakuti ndiwo moyo wa: nyama zonse, mwazi wace ndiwo moyo wace; cifukwa cace ndinanena kwa ana a Israyeli, Musamadya mwazi wa nyama iri yonse; pakuti moyo wa nyama yonse ndi mwazi wace; ali yense akaudya adzasadzidwa.
15 Ndipo ali yense wakudya yakufa yokha, kapena yojiwa kuthengo, ngakhale ndiye wa m'dziko kapena mlendo, azitsuka nsaru zace, nasambe ndi madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo; pamenepo adzakhala woyera.
16 Koma akapanda kuzitsuka, kapena kusamba thupi lace, adzasenza mpholupulu yace.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Ine ndine Yehova Molungu wanu.
3 Musamacita monga mwa macitidwe a dziko la Aigupto muja munakhalamo; musamacita monga mwa macitidwe a dziko la Kanani kumene ndipita nanuko, nimusamayenda m'malemba ao.
4 Muzicita maweruzo anga, ndi kusunga malemba anga, kumayenda m'mwemo; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5 Inde, muzisunga malemba anga, ndi maweruzo anga; amenewo munthu akawacita, adzakhala nao ndi moyo; Ine ndine Yehova.
6 Asasendere mmodzi wa inu kwa mbale wacekumbvula; Ine ndine Yehova.
7 Usamabvula atate wako, ndi mai wako; ndiye mai wako, usamambvula.
8 Usamabvula mkazi wa atate wako; ndiye thupi la atate wako.
9 Usamabvula mlongo wako, mwana wamkazi wa atate wako, kapena mwana wamkazi wa mai wako, wobadwa kwanu, kapena wobadwa kwina.
10 Usamabvula mwana wamkazi wa mwana wamwamuna wako, kapena mwana wamkazi wa mwana wamkazi wako; pakuti thupi lao ndi lako.
11 Usamabvula mwana wamkazi wa mkazi wa atate wako, amene anambala atate wako, ndiye mlongo wako.
12 Usamabvula mlongo wa atate wako; ndiye wa cibale ca atate wako.
13 Usamabvula mbale wa mai wako; popeza ndiye mbale wa mai wako.
14 Usamabvula mbale wa atate wako; usamasendera kwa mkazi wace; ndiye mai wako.
15 Usamabvula mpongozi wako; ndiye mkazi wa mwana wamwamuna wako; usamambvula.
16 Usamabvula mkazi wa mbale wako; ndiye thupi la mbale wako.
17 Usamabvula mkazi ndi mwana wamkazi wace; usamatenga mwana wamkazi wa mwana wamwamuna wace, kapena mwana wamkazi wa mwana wamkazi wace kumbvula; ndiwo abale; cocititsa manyazi ici.
18 Usamtenga mkazi kumuonjezera kwa mbale wace, kumbvuta, kumbvula pamodzi ndi mnzace, akah ndi moyo mnzaceyo.
19 Usamasendera kwa mkazi kumbvula pokhala ali padera cifukwa ca kudetsedwa kwace.
20 Usagona naye mkazi wa mnansi wako, kudetsedwa naye limodzi.
21 Ndipo usamapereka a mbumba yako kuwapitiriza kumoto cifukwa ca Moleke, usamaipsa dzina la Mulungu wako: Ine ndine Yehova.
22 Usamagonana ndi mwamuna, monga amagonana ndi mkazi; conyansa ici.
23 Ndipo usamagonana ndi nyama iri yonse, kudetsedwa nayo; kapena mkazi asamaima panyama, kugonana nayo; cisokonezo coopsa ici.
24 Musamadzidetsa naco cimodzi ca izi; pakuti amitundu amene ndiwapitikitsa pamaso panu amadetsedwa nazo zonsezi;
25 dziko lomwe lidetsedwa; cifukwa cace ndililanga, ndi dzikoli lisanza okhala m'mwemo.
26 Koma inu, muzisunga malemba anga ndi maweruzo anga, osacita cimodzi conse ca zonyansa izi; ngakhale wa m'dziko ngakhale mlendo wakugonera pakati pa inu;
27 (pakuti eni dziko okhalako, musanafike inu, anazicita zonyansa izi zonse, ndi dziko linadetsedwa)
28 lingakusanzeni inunso dzikoli, polidetsa inu, monga linasanza mtundu wa anthu wokhalako musanafike inu.
29 Pakuti ali yense akacita ciri conse ca zonyansa Izi, inde amene azicita idzasadzidwa pakati pa anthu a mtundu wao.
30 Potero muzisunga cilangizo canga, ndi kusacita ziri zonse za miyambo yonyansayi anaicita musanafike inu, ndi kusadzidetsa nayo: Ine ndine Yehova Mulungu-wako.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2 Nena ndi khamu lonse la ana a Israyeli, nuti nao, Muzikhala oyera; pakuti ine ndine Yehova Mulungu wanu, ndine woyera.
3 Ali yense aopemai wace, ndi atate wace; nimusunge masabata anga; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
4 Musamatembenukira mafano, kapena kudzipangira mulungu woyenga; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
5 Ndipo pamene muphera Yehova nsembe yoyamika, muiphere kuti mulandiridwe.
6 Tsiku lomwelo mwaipha, ndi m'mawa mwace muidye; ngati katsalirako kanthu tsiku lacitatu, muzikatentha ndi moto.
7 Akakadya konse tsiku tacitatu kali conyansa, kosabvomerezeka:
8 koma ali yense akudyako adzasenza mphulupulu yace, popeza waipsa copatulidwa ca Yehova; ndi munthuyo amsadze, kumcotsa kwa anthu a mtundu wace.
9 Pakukolola dzinthu za m'dziko mwanu, usamakololetsa m'mphepete mwa munda wako, nusamakunkha khunkha.
10 Usamakunkha khunkha la m'munda wako wamphesa, usamazitola zidagwazi za m'munda wako wamphesa; uzisiyire wosauka ndi mlendo; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
11 Musamaba, kapena kunyenga, kapena kunamizana.
12 Musamalumbira monama ndi kuchula dzina langa, ungaipse dzina la Mulungu wako; Ine ndine Yehova.
13 Usamasautsa mnansi wako, kapena kulanda zace; mphotho yace ya wolipidwa isakhale ndi iwe kufikira m'mawa.
14 Usamatemberera wogontha; usamaika cokhumudwitsa pamaso pa wosaona; koma uziopa Mulungu wako; Ine ndine Yehova.
15 Musamacita cisalungamo pakuwemza mlandu; usamabvomereza munthu wosauka, kapena kulemekeza munthu womveka; uweruze mlandu wa munthu mnzako molungama.
16 Usamayendayenda nusinjirira mwa anthu a mtundu wako; usamatsata mwazi wa mnansi wako; Ine ndine Yehova.
17 Usamamuda mbale wako mumtima mwako; umdzudzule munthu mnzako ndithu, usadzitengera ucimo cifukwa ca iye.
18 Usamabwezera cilango, kapena kusunga kanthu kukhosi pa ana a anthu a mtundu wako; koma uzikonda mnansi wako monga udzikonda wekha; Ine ndine Yehova.
19 Muzisunga malemba anga, Usamalola zoweta zako za mitundu yosiyana zikwerane; usamabzala m'munda mwako mbeu za mitundu iwiri; usamabvala cobvala ca nsaru za mitundu iwiri zosokonezana.
20 Munthu akagona ndi mkazi, ndiye mdzakazi, wopalidwa ubwenzi ndi mwamuna, wosamuombola kapena wosapatsidwa ufulu, akwapulidwe; asawaphe, popeza si mfulu mkaziyo.
21 Ndipo adze nayo nsembe yace yoparamula kwa Yehova, ku khomo la cihema cokomanako, ndiyo nkhosa yamphongo ikhale nsembe yoparamula.
22 Ndipo wansembe acite comtetezera ndi nkhosa yamphongo ya nsembe yoparamula pamaso pa Yehova, cifukwa ca kucimwa adacimwaku; ndipo adzakhululukidwa cifukwa ca kucimwa kwace adacimwaku.
23 Ndipo mukadzalowa m'dzikomo, ndi kubzalamitengo yamitundumitundu ikhale ya cakudya, muziyese zipatso zao monga kusadulidwa kwao; zaka zitatu muziyese zosadulidwa; zisadyedwa.
24 Koma caka cacinai zipatso zace zonse zikhale zopatulika, za kumlemekeza nazo Yehova.
25 Caka cacisanu muzidya zipatso zace, kuti zobala zace zikucurukireni inu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
26 Musamadya kanthu ndi mwazi wace; musamacita nyanga, kapena kuombeza ula.
27 Musamameta mduliro, kapena kusenga m'mphepete mwa ndebvu zanu,
28 Musamadziceka matupi anu cifukwa ca akufa, kapena kutema mpbini; Ine ndine Yehova.
29 Usamaipsa mwana wako wamkazi ndi kumcititsa cigololo; lingadzale ndi cigololo dzikoli, ndi kudzazidwa nazo zocititsa manyazi.
30 Muzisunga masabata anga, ndi kucitira ulemu malo anga opatulika; Ine ndine Yehova.
31 Musamatembenukira kwa obwebweta, kapena anyanga; musawafuna, ndi kudetsedwa nao; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
32 Pali aimvi uziwagwadira, nucitire ulemu munthu wokalamba; nuope Mulungu wako; lnendine Yehova.
33 Ndipo mlendo akagonera m'dziko mwanu, musamamsautsa.
34 Mlendo wakugonera kwa inu mumuyese pakati pa inu monga wa m'dziko momwemo; umkonde monga udzikonda wekha; popeza munali alendo m'dziko la Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
35 Musamacita cisalungamo poweruza mlandu, poyesa utali wace, kulemera kwace, kapena kucuruka kwace.
36 Mukhale naco coyesera coona, miyeso yoona, era woona, bini woona; Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakuturutsani m'dziko la Aigupto.
37 Ndipo musamalire malemba anga onse, ndi maweruzo anga onse, ndi kuwacita; Ine ndine Yehova.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2 Unenenso kwa ana a Israyeli ndi kuti, Ali yense wa ana a Israyeli, kapena wa alendo akukhala m'Israyeli, amene apereka mbeu zace kwa Moleke, azimupha ndithu; anthu a m'dziko amponye miyala.
3 Ndipo nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndi kumsadza kumcotsa pakati pa anthu a mtundu wace; popeza anapereka a mbeu zace kwa Moleke, kudetsa nako malo anga opatulika, ndi kuipsa dzina langa lopatulika.
4 Ndipo ngati anthu a m'dzikomo akambisa munthuyo pang'ono ponse, pamene apereka a mbeu zace kwa Moleke, kuti asamuphe;
5 pamenepo nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndi banja lace, ndi kumsadza iye, ndi onse akumtsata ndi cigololo kukacita cigololo kwa Moleke, kuwacotsa pakati pa anthu a mtundu wao.
6 Ndipo munthu wakutembenukira kwa obwebweta ndi anyanga kuwatsata ndi cigololo, nkhope yanga idzatsutsana naye munthuyo, ndipo ndidzamsadza kumcotsa pakati pa anthu a mtundu wace.
7 Cifukwa cace dzipatuleni, nimukhale oyera; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
8 Ndipo musunge malemba anga ndi kuwacita; Ine ndine Yehova wakupatula inu.
9 Pakuti ali yense wakutemberera atate wace kapena mai wace azimupha ndithu; watemberera atate wace kapena mai wace; mwazi wace ukhale pamutu pace.
10 Munthu akacita cigololo ndi mkazi wa mwini, popeza wacita cigololo ndi mkazi wa mnansi wace, awaphe nditho, mwamuna ndi mkazi onse awiri.
11 Munthu akagona naye mkazi wa atate wace, wabvula atate wace; awaphe ndithu onse awiri; mwazi wao ukhale pamtu pao.
12 Munthu akagona ndi mpongozi wace, awaphe onse awiri; acita cisokonezo; mwazi wao ukhale pamtu pao.
13 Munthu akagonana ndi mwamuna mnzace, monga amagonana ndi mkazi, acita conyansa onse awiri; awaphe ndithu; mwazi wao ukhale pamtu pao.
14 Munthu akatenga mkazi pamodzi ndi mai wace cocititsa manyazi ici; aziwatentha ndi moto, iye ndi iwowa; kuti pasakhale cocititsa manyazico pakati pa inu.
15 Mwamuna akagona ndi nyama amuphe ndithu; muiphenso nyamayi.
16 Mkazi akasendera kwa nyama iri yonse kugonana nayo, umuphe mkaziyo, ndi nyama yomwe; muwaphe ndithu; mwazi wao ukhale pamtu pao.
17 Munthu akatenga mlongo wace, mwana wamkazi wa atate wace, kapena mwana wamkazi wa mai wace, nakaona thupi lace, ndi mlongoyo akaona thupi lace; cocititsa manyazi ici; ndipo awasadze pamaso pa ana a anthu ao; anabvula mlongo wace; asenze mphulupulu yace.
18 Munthu akagona ndi mkazi ali mumsambo, nakambvula, anabvula kasupe wace, ndi iye mwini anabvula kasupe wa nthenda yace; awadule onse awiri pakati pa anthu a mtundu wao.
19 Usamabvula mbale wa mai wako, kapena mlongo wa atate wako; popeza anabvula abale ace; asenze mphulupulu yao.
20 Munthu akagona ndi mkazi wa mbale wa atate wace, nabvula mbale wa atate wace; asenze kucimwa kwao; adzafa osaona ana.
21 Munthu akatenga mkazi wa mbale wace, codetsa ici; wabvula mbale wace; adzakhala osaona ana.
22 Potero muzisunga malemba anga onse, ndi maweruzo anga onse, kuwacita; lingakusanzeni inu dziko limene ndipita nanuko, kuti mukhale m'mwemo.
23 Musamatsata miyambo ya mtundu umene neliucotsa pamaso panu; popeza anacita izi zonse, nelinalema nao.
24 Koma ndanena nanu, Mudzalandira dziko lao inu, ndipo Ine ndilipereka kwa inu likhale lanu, ndilo dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi; Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakusiyanitsani ndi mitundu yina ya anthu.
25 Potero musiyanitse pakati pa nyama zoyera ndi nyama zodetsa, ndi pakati pa mbalame zodetsa ndi zoyera; ndipo musadzinyansitsa ndi nyama, kapena mbalame, kapena ndi kanthu kali konse kakukwawa pansi, kamene ndinakusiyanitsirani kakhale kodetsa.
26 Ndipo muzikhala oyera kwa Ine; pakuti Ine Yehova ndine woyera, ndipo ndinakusiyanitsani kwa mitundu ya anthu mukhale anga.
27 Munthu wamwamuna kapena wamkazi wakubwebweta, kapena wanyanga, azimupha ndithu; aziwaponya miyala; mwazi wao ukhale pamtu pao.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Nena ndi ansembe, ana a Aroniwo, nuti nao, Asadzidetse mmodzi wa inu cifukwa ca wakufa mwa anthu a mtundu wace;
2 koma cifukwa ca abale ace eni eni ndiwo, mai wace, ndi atate wace, ndi mwana wace wamwamuna, ndi mwana wace wamkazi, ndi mbale wace;
3 ndi cifukwa ca mlongo wace weni weni, akakhala namwali wosakhala naye mwamuna, nkuloleka adzidetse cifukwa ca iwowa.
4 Akakhala mwini banja pakati pa anthu a mtundu wace, asadzidetse, ndi kudziipsa,
5 Asamete tsitsi la pamtu pao, kapena kucecerera ndebvu zao, kapena kudziceka matupi ao.
6 Azikhala opatulikira Mulungu wao, osaipsa dzina la Mulungu wao; popeza amapereka nsembe zamoto za Yehova, mkate wa Mulungu wao; cifukwa cace akhale opatulika.
7 Asadzitengere mkazi wacigololo, kapena woipsidwa; asatenge mkazi woti adamcotsa mwamuna wace; popeza apatulikira Mulungu wace.
8 Cifukwa cace umpatule; popeza amapereka mkate wa Mulungu wako; umuyese wopatulika; pakuti Ine Yehova wakupatula iwe, ndine woyera,
9 Akadziipsa mwana wamkazi wa wansembe ndi kucita cigololo, alikuipsa atate wace; amtenthe ndi moto.
10 Ndipo iye wokhala mkulu wansembe mwa abale ace, amene anamtsanulira mafuta odzoza pamutu pace, amene anamdzaza dzanja kuti abvale zobvalazo, asawinde, kapena kung'amba zobvala zace.
11 Asafike kuli mtembo; asadzidetse cifukwa ca atate wace, kapena mai wace.
12 Asaturuke m'malo opatulika, kapena kuipsa malo opatulika a Mulungu wace; popeza korona wa mafuta odzoza wa Mulungu wace ali pa iye; Ine ndine Yehova.
13 Ndipo adzitengere mkazi akali namwali.
14 Mkazi wamasiye, kapena womleka, kapena woipsidwa, wacigololo, oterewa asawatenge; koma azitenga namwali wa anthu a mtundu wace akhale mkazi wace.
15 Asaipse mbeu yace mwa anthu a mtundu wace; popeza Ine ndine Yehova wakumpatula iye.
16 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
17 Nena ndi Aroni, kuti, Ali yense wa mbeu zako mwa mibadwo yao wakukhala naco cirema, asayandikize kupereka mkate wa Mulungu wace.
18 Pakuti munthu ali yense wokhala naco cirema, asayandikize; wakhungu, kapena wotsimphina, kapena wopunduka mph uno, kapena wamkuru ciwalo,
19 kapena munthu wopunduka phazi kapena wopunduka dzanja,
20 kapena wowerama, kapena wamfupi msinkhu, kapena wopunduka diso, kapena munthu wamphere, kapena wacipere, kapena wopunduka kumoto.
21 Wa mbeu ya Aroni wansembe asayandikize mmodzi wokhala naco cirema, kupereka nsembe zamoto za Yehova; ali naco cirema asayandikize kupereka cakudya ca Mulungu wace.
22 Adye cakudya ca Mulungu wace, copatulikitsa, ndi copatulika;
23 koma asafike ku nsaru yocinga, asayandikize ku guwa la nsembe, popeza ali naco cirema; kuti angaipse malo anga opatulika; popeza Ine ndine Yehova wakuwapatula.
24 Momwemo Mose ananena ndi Aroni, ndi ana ace amuna, ndi ana onse a Israyeli.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2 Nena ndi Aroni ndi ana ace amuna, kuti azikhala padera ndi zinthu zopatulika za ana a Israyeli, zimene amandipatulira Ine, ndipo asaipse dzina langa loyera; Ine ndine Yehova.
3 Nena nao, Ali yense wa mbeu zanu zonse mwa mibadwo yanu, akayandikiza zinthu zopatulika, zimene ana a Israyeli azipatulira Yehova, pokhala ali naco comdetsa cace, azimsadza munthuyo pankhope panga; Ine ndine Yehova.
4 Munthu ali yense wa mbeu za Aroni wokhala ndi khate, kapena kukha, asadyeko zinthu zopatulika, kufikira atayera. Ndipo ali yense wokhudza cinthu codetsedwa ndi wakufa, kapena mwamuna wogona uipa;
5 ndi ali yense wokhudza cinthu cokwawa cakudetsedwa naco, kapenanso munthu amene akamdetsa naco, codetsa cace ciri conse;
6 munthu wokhudza ciri conse cotere adzakhala wodetsedwa kufikira madzulo, ndipo asadye zinthu zopatulika, akapanda kusamba thupi lace ndi madzi.
7 Koma litalowa dzuwa, adzakhala woyera, ndi pambuyo pace adyeko zoyerazo, popeza ndizo cakudya cace.
8 Asamadya zakufa zokha, kapena zojiwa, kudzidetsa nazo; Ine ndine Yehova.
9 Potero asunge cilangizo canga, angasenzepo ucimo, ndi kufera m'mwemo, pakuciipsa; Ine ndine Yehova wakuwapatula iwo,
10 Mlendo asadyeko copatulikaco; wakungokhala, ndi wansembe, kapena wolembedwa nchito, asadyeko copatulikaco.
11 Koma wansembe atakagula munthu ndi ndarama zace, iyeyu adyeko; ndi iwo amene anabadwa m'nyumba yace, adyeko mkate wace.
12 Ndipo mwana wamkazi wa wansembe akakwatibwa ndi mlendo, asadyeko nsembe yokweza ya zinthu zopatulika.
13 Koma mwana wamkazi wa wansembe akakhala wamasiye kapena wocotsedwa, ndipo alibe mwana, nabwerera ku nyumba ya atate wace, monga muja anali mwana, adyeko mkate wa atate wace; koma mlendo asamadyako.
14 Ndipo munthu akadyako cinthu copatulika mosadziwa, azionjezapo limodzi la magawo asanu, nalipereke kwa wansembe, pamodzi ndi copatulikaco.
15 Potero asaipse zinthu zopatulika za ana a Israyeli, zopereka iwo kwa Yehova;
16 ndi kuwasenzetsa mphulupulu yakuwaparamulitsa, pakudya iwo zopatulika zao; pakuti Ine ndine Yehova wakuwapatula.
17 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
18 Nena ndi Aroni, ndi ana ace amuna, ndi ana onse a Israyeli, nuti nao, Ali yense wa mbumba ya Israyeli, kapena wa alendo ali m'Israyeli, akabwera naco copereka cace, monga mwa zowinda zao zonse, kapena monga mwa zopereka zaufulu zao, zimene abwera nazo kwa Yehova zikhale nsembe zopsereza;
19 kuti mulandiridwe, azibwera navo yaimuna yopanda cirema, ya ng'ombe, kapena nkhosa, kapena mbuzi.
20 Musamabwera nayo yokhala ndi cirema; popeza siidzalandirikira inu.
21 Ndipo munthu akabwera nayo nsembe yoyamika kwa Yehova, ya pa cowinda cacikuru, kapena ya pa copereka caufulu, ya ng'ombe kapena nkhosa, ikhale yangwiro kuti ilandirike; ikhale yopanda cirema.
22 Musamabwera nazo kwa Yehova yakhungu, kapenayodukamwendokapena yopunduka, kapena yapfundo, kapena yausemwe, kapena ya usemwe waukuru, musamazipereka kwa Yehova nsembe zamoto pa guwa la nsembe.
23 Ng'ombe kapena nkhosa yokula kapena yocepa ciwalo, ikhale nsembe yaufulu; koma pa cowinda siidzalandirika.
24 Nyama yofula, kapena copwanya kapena cosansantha, kapena cotudzula, kapena codula, musamabwera nazo kwa Yehova; inde musamacicita ici m'dziko mwanu.
25 Ndipo musamazilandira izi ku dzanja la mlendo ndi kubwera nazo zikhale cakudya ca Mulungu wanu; popeza ziri nako kubvunda kwao; ziri ndi cirema; sizidzalandirikira inu.
26 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti, Zikamabadwa ng'ombe kapena nkhosa, kapena mbuzi, zikhale ndi mace masiku asanu ndi awiri;
27 kuyambira tsiku lacisanu ndi citatu ndi m'tsogolo mwace, idzalandirika ngati copereka nsembe yamoto ya Yehova.
28 Koma musamaipha ng'ombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wace tsiku limodzimodzi.
29 Ndipo mukamaphera Yehova nsembe yoyamika, muiphere kuti mulandirike.
30 Idyedwe tsiku lomwelo; musamasiyako kufikira m'mawa; Ine ndine Yehova.
31 Potero muwasunge malamulo anga, ndi kuwacita; Ine ndine Yehova.
32 Musamaipsa dzina langa loyera; koma ndikhale woyera pakati pa ana a Israyeli; Ine ndine Yehova wakukupatulani,
33 amene ndinakuturutsani m'dziko la Aigupto, kuti ndikhale Mulungu wanu; Ine ndine Yehova.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Nyengo zoikika za Yehova zimene muzilalikira zikhale masonkhano opatulika, ndizo nyengo zanga zoikika.
3 Masiku asanu ndi limodzi azigwira nchito; koma lacisanu ndi ciwiri ndilo Sabata lakupumula, msonkhano wopatulika; musamagwira nchito konse; ndilo sabata la Yehova m'nyumba zanu zonse.
4 Izi ndi nyengo zoikika za Yehova, masonkhano opatulika, zimene muzilalikira pa nyengo zoikika zao.
5 Mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi cinai la mweziwo, madzulo, pali Paskha wa Yehova.
6 Ndipo tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi womwewo ndilo madyerero a mkate wopanda cotupitsa a Yehova; masiku asanu ndi awiri muzidya mkate wopanda cotupitsa.
7 Tsiku lace loyamba mukhale nao msonkhano wopatulika; musamagwira nchito ya masiku ena.
8 Koma mubwere nayo kwa Yehova nsembe yamoto masiku asanu ndi awiri; pa tsiku lacisanu ndi ciwiri pakhale msonkhano wopatulika; musamacita nchito ya masiku ena.
9 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
10 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mutakalowa m'dziko limene ndikupatsani, ndi kuceka dzinthu zace, pamenepo muzidza nao mtolo wa zipatso zoyamba za masika anu kwa wansembe;
11 ndipo iye aweyule mtolowo pamaso pa Yehova, ulandirikire inu, tsiku lotsata sabata wansembe aweyule.
12 Ndipo tsiku loweyula mtolowo, ukonze mwana wa nkhosa wopanda cirema, wa caka cimodzi, akhale nsembe yopsereza ya Yehova.
13 Ndipo nsembe yaufa yace ikhale awiri a magawo khumi a ufa wosalala wosanganiza ndi mafuta, ndiyo nsembe yamoto ya Yehova, icite pfungo lokoma; ndi nsembe yace yothira ikhale yavinyo, limodzi la magawo anai la hini.
14 Musamadya mkate, kapena tirigu wokazinga, kapena ngala zaziwisi, kufikira tsiku lomweli, kufikira mutadza naco copereka ca Mulungu wanu; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu m'nyumba zanu zonse.
15 Ndipo mudziwerengere kuyambira tsiku lotsata Sabata, kuyambira tsikuli mudadza nao mtolo wa nsembe yoweyula; pakhale masabata asanu ndi awiri amphumphu;
16 muwerenge masiku makumi asanu kufikira tsiku lotsata sabata lacisanu ndi ciwiri; pamenepo mubwere nayo kwa Yehova nsembe ya ufa watsopano.
17 Muturuke nayo m'zinyumba zanu mikate iwiri ya nsembe yoweyula, ikhale ya awiri a magawo khumi a efa; ikhale ya ufa wosalala, yopanga ndi cotupitsa, zipatso zoyamba za Yehova.
18 Ndipo mubwere nao pamodzi ndi mikate, ana a nkhosa asanu ndi awiri, opanda cirema a caka cimodzi, ndi ng'ombe yamphongo imodzi, ndi nkhosa zamphongo ziwiri; zikhale nsembe yopsereza ya Yehova, pamodzi ndi nsembe yao yaufa, ndi nsembe zao zothira, ndizo nsembe yamoto ya pfungo lokoma la Yehova.
19 Mukonzenso mwana wa mbuzi mmodzi akhale nsembe yaucimo, ndi ana a nkhosa awiri a caka cimodzi akhale nsembe yoyamika.
20 Ndi wansembe awaweyule, pamodzi ndi mkate wa zipatso zoyamba, nsembe yoweyula pamaso pa Yehova, pamodzi ndi ana a nkhosa awiriwo; zikhale zopatulikira Yehova, kuti zikhale za wansembe.
21 Ndipo mulalikire tsiku lomwelo; kuti mukhale nao msonkhano wopatulika; musamagwira nchito ya masiku ena; ndilo lemba losatha m'nyumba zanu zonse, mwa mibadwo yanu yonse.
22 Ndipo pakukolola dzinthu za m'dziko mwanu, usamakololetsa m'mphepete mwa munda wako, nusamakunkha khunkha; uzisiyire wosauka ndi mlendo; Ine ndine Yehova Mulungu wako.
23 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
24 Nena ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku loyamba la mweziwo, muzipumula, ndiko cikumbutso ca kuliza malipenga, msonkhano wopatulika.
25 Musamagwira nchito ya masiku ena; mubwere nayo nsembe yamoto ya Yehova.
26 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
27 Komatu, tsiku lakhumi la mwezi uwu wacisanu ndi ciwiri, ndilo tsiku la citetezero; mukhale nao msonkhano wopatulika, ndipo mudzicepetse; ndi kubwera nayo nsembe yamoto kwa Yehova.
28 Musamagwira nchito iri yonse tsiku limenelo; pakuti ndilo tsiku la citetezero, kucita cotetezera inu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 Pakuti munthu ali yense wosadzicepetsa tsiku limenelo, amsadze kwa anthu a mtundu wace.
30 Ndi munthu ali yense wakugwira nchito iri yonse tsiku limenelo, ndidzaononga munthuyo pakati pa anthu a mtundu wace.
31 Musamagwira nchito iri yonse; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu, m'nyumba zanu zoo nse.
32 Likhale ndi inu Sabata lakupumula; ndipo mudzicepetse; tsiku lacisanu ndi cinai madzulo, kuyambira madzulo kufikira madzulo musunge Sabata lanu.
33 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
34 Nena ndi ana a Israyeli, kuti, Tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi uno wacisanu ndi ciwiri pali madyerero a misasa a Yehova, masiku asanu ndi awiri.
35 Tsiku loyamba likhale msonkhano wopatulika, musamagwira nchito ya masiku ena.
36 Masiku asanu ndi awiri mubwere nayo nsembe yamoto kwa Yehova; tsiku lacisanu ndi citatu mukhale nao msonkhano wopatulika; ndipo mubwere nayo nsembe yamoto kwa Yehova; ndilo lotsirizira; musamagwira nchito ya masiku ena.
37 Izi ndi nyengo zoikika za Yehova, zimene muzilalikira zikhale masonkhano opatulika, kukabwera nayo nsembe yamoto kwa Yehova, nsembe yopsereza, ndi nsembe yaufa, nsembe yophera, ndi nsembe yothira, yonse pa tsiku lace lace;
38 pamodzi ndi masabata a Yehova, ndi pamodzi ndi mphatso zanu, ndi pamodzi ndi zoo winda zanu zonse, ndi pamodzi ndi zopereka zaufulu zanu, zimene muzipereka kwa Yehova.
39 Koma tsiku lakhumi ndi cisanu la mwezi wacisanu ndi ciwiri, mutatuta zipatso za m'dziko, muzisunga madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri; tsiku loyamba mupumule, ndi tsiku lacisanu ndi citatu mupumule.
40 Ndipo tsiku loyambali mudzitengere nthambi za mitengo yokoma, nsomo za kanjedza, ndi nthambi za mitengo yobvalira, ndi misondodzi ya kumtsinje; ndipo mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu masiku asanu ndi awiri.
41 Ndipo muwasunge madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri m'caka; ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu; musunge mwezi wacisanu ndi ciwiri.
42 Mukhale m'misasa masiku asanu ndi awiri; onse obadwa m'dziko mwa Israyeli akhale m'misasa;
43 kuti mibadwo yanu ikadziwe lruti ndinakhalitsa ana a Israyeli m'misasa, pamene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
44 Ndipo Mose anafotokozera ana a Israyeli nyengo zoikika za Yehova.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2 Uza ana a Israyeli, kuti akutengere mafuta a azitona oyera opera akuunikira, kuti aziwalitsa nyali nthawi zonse.
3 Aroni aikonze kunja kwa nsaru yocinga ya mboni, m'cihema cokomanako, kuyambira madzulo kufikira m'mawa, pamaso pa Yehova nthawi zonse; likhale lemba losatha mwa mibadwo yanu.
4 Akonze nyalizo pa coikapo nyali coona pamaso pa Yehova nthawi zonse.
5 Ndipo uzitenga ufa wosalala, ndi kuphika timitanda khumi ndi tiwiri; awiri a magawo khumi a efa afikane kamtanda kamodzi,
6 Ndipo utiike m'mizere iwiri, tisanu ndi kamodzi mzere umodzi, pa gome loyera, pamaso pa Yehova.
7 Nuike libano loona ku mzere uli wonse, kuti likhale kumkate ngati cokumbutsa, nsembe yamoto ya Yehova.
8 Nthawi zonse tsiku la Sabata aukonze pamaso pa Yehova, cifukwa ca ana a Israyeli, ndilo pangano losatha.
9 Ndipo ukhale wa Aroni ndi ana ace, audye pamalo popatulika; pakuti auyese wopatulikitsa wocokera ku nsembe zamoto za Yehova; ndilo lemba losatha.
10 Ndipo mwana wamwamuna wa mkazi M-israyeli, atate wace ndiye M-aigupto, anaturuka mwa ana a Israyeli; ndi mwana wamwamuna wa mkazi M-israyeliyo analimbana naye munthu M-israyeli kucigono;
11 ndipo mwana wamwamuna wa mkazi M-israyeli anacitira DZINA mwano, natemberera; ndipo anadza naye kwa Mose. Dzina la mai wace ndiye Selomiti, mwana wa Dibri, wa pfuko la Dani.
12 Ndipo anamsunga m'kaidi, kuti awafotokozere m'mene anenere Yehova.
13 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
14 Turuka naye wotembererayo kunja kwa cigono; ndipo onse adamumva aike manja ao pamutu pace, ndi khamu lonse limponye miyala afe.
15 Ndipo unene ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Ali yense wotemberera Mulungu wace azisenza kucimwa kwace.
16 Ndi iye wakucitira mwano dzina la Yehova, amuphe ndithu; khamu lonse limponye miyala ndithu; mlendo ndi wobadwa m'dziko yemwe akacitira dzina la Yehova mwano, awaphe.
17 Munthu akakantha munthu mnzace ali yense kuti afe, amuphe ndithu.
18 Munthu akakantha nyama kuti ife, ambwezere yina; moyo kulipa moyo.
19 Munthu akacititsa mnansi wace cirema, monga umo anacitira momwemo amcitire iye;
20 kutyola kulipa kutyola, diso kulipa diso, dzino kulipa dzino; monga umo anacitira munthu cirema, momwemo amcitire iye.
21 Iye wakukantha nyama kuti ife, ambwezere yina; iye wakupha munthu, amuphe.
22 Ciweruzo canu cifanefane ndi mlendo ndi wobadwa m'dziko; pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
23 Ndipo Mose ananena ndi ana a Israyeli, ndipo anaturutsa wotembererayo kunja kwa cigono, namponya miyala. Ndipo ana a Israyeli anacita monga Yehova adauza Mose.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'phiri la Sinai, ndi kuti,
2 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mutakalowa m'dziko limene ndikupatsani, dzikoli lizisungira Yehova Sabata.
3 Zaka zisanu ndi cimodzi ubzale m'munda mwako, ndi zaka zisanu ndi cimodzi udzombole mphesa zako, ndi kuceka zipatso zace;
4 koma caka cacisanu ndi ciwiri cikhale sabata lakupumula la dziko, sabata la Yehova; usamabzala m'munda mwako, usamadzombola mipesa yako.
5 Zophuka zokha zofikira masika usamazichera, ndi mphesa za mipesa yako yosadzombola usaziceka; cikhale caka copumula dziko.
6 Ndipo sabata la dzikoli likhale kwa inu la cakudya; kwa iwe, ndi mnyamata wako, ndi mdzakazi wako, ndi wolembedwa nchito yako, ndi mlendo wako wakugonera kwanu;
7 ndi ng'ombe zako, ndi nyama ziri m'dziko lako; zipatso zace zonse zikhale cakudya cao.
8 Ndipo uziwerengera masabata a zaka asanu ndi awiri, zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawiri; kotero kuti zaka za masabata a zaka asanu ndi awiri, zifikire zaka makumi anai kudza zisanu ndi zinai.
9 Pamenepo uzitumizira lipenga lomveka m'mwezi wacisanu ndi ciwiri, tsiku lakhumi la mweziwo; tsiku la citetezero mutumizire lipenga lifikire m'dziko lanu lonse.
10 Ndipo mucipatule caka ca makumi asanu, ndi kulalikira kwa onse okhala m'dzikomo kuti akhale aufulu; muciyese caka coliza lipenga; ndipo mubwerere munthu ali yense ku zace zace, ndipo mubwerere yense ku banja lace.
11 Muciyese caka ca makomi asanuco coliza lipenga, musamabzala, kapena kuceka zophuka zokha m'mwemo; kapenakuceka mphesa zace za mipesa yosadzombola.
12 Popeza ndico caka coliza lipenga; muciyese copatulika, mudye zipatso zace kunja kwa munda.
13 Caka coliza lipenga ici mubwerere nonse ku zace zace.
14 Ndipo ukagulitsa kanthu kwa mnansi wako, kapena kugula kanthu ka mnansi wako, musamasautsana;
15 monga mwa kuwerenga kwace kwa zaka, citapita coliza lipenga, uzigula kwa mnansi wako, ndi monga mwa kuwerenga kwa zaka za zipatso azigulitsa.
16 Monga mwa kucuruka kwa zaka zace uonjeze mtengo wace, ndi monga mwa kucepa kwa zaka zace ucepse mtengo wace; pakuti akugulitsa powerenga masiku ace.
17 Musamasautsana, koma uope Mulungu wako; popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
18 M'mwemo mucite malemba anga, ndi kusunga maweruzo anga, ndi kuwacita; ndipo mudzakhala m'dzikomo okhazikika.
19 Dziko lidzaperekanso zipatso zace, ndipo mudzadya ndi kukhuta, ndi k'ukhalamo okhazikika.
20 Ndipo mukadzati, Tidzadyanji caka cacisanu ndi ciwiri? taonani, sitidzabzala, sitidzakolola dzinthu;
21 pamenepo ndidzauza dalitso langa litsike pa inu caka cacisanu ndi cimodzi, ndipo cidzapatsa zipatso zofikira zaka zitatu.
22 Ndipo mubzale caka cacisanu ndi citatu, ndi kudya zipatso zasundwe; kufikira caka cacisanu ndi cinai, mpaka zitacha zipatso zace mudzadya zasundwe.
23 Ndipo asaligulitse dziko cigulitsire; popeza dzikoli ndi langa; pakuti inu ndinu alendo akugonera ndi Ine.
24 Potero muzilola liomboledwe dziko lonse muli nalo.
25 Mbale wako akasaukira cuma, nakagulitsa cace cace, pamenepo mombolo wace, mbale wace weni weni azidza, naombole cimene mbale wace anagulitsaco.
26 Ndipo munthu akasowa mombolo, koma dzanja lace lacionetsa, nacipeza cofikira kuciombola;
27 pamenepo awerenge zaka za kugulitsa kwace, nabwezere wosulayo zotsalirapo, nabwerere iye ku dziko lace.
28 Koma dzanja lace likapanda kupeza zofikira za kumbwezera, pamenepo cogulitsaco cikhale m'dzanja lace la iye adacigulayo, kufikira caka coliza lipenga; koma caka coliza lipenga cituruke, nabwerere iye ku dziko lace.
29 Munthu akagulitsa nyumba yogonamo, m'mudzi wa m'linga, aiombole cisanathe caka coigulitsa; kufikira kutha caka akhoza kuombola.
30 Ndipo akapanda kuiombola kufikira kutha kwace kwa caka camphumphu, nyumba iri m'mudzi wa m'lingayi idzakhala yace ya iye adaigula yosamcokeranso mwa mibadwo yace; siidzaturuka caka coliza lipenga.
31 Koma nyumba za m'midzi yopanda linga aziyese monga minda ya m'dziko; ziomboledwe, zituruke m'caka coliza lipenga.
32 Kunena za midzi ya Alevi, nyumba za m'midzi yao yao, Alevi akhoza kuziombola nthawi zonse.
33 Ndipo munthu akagula kwa Mlevi, nyumba yogulayo yokhala m'mudzi wace wace, ituruke m'caka coliza lipenga, popeza nyumba za m'midzi ya Alevi ndizo zao zao mwa ana a Israyeli.
34 Koma dambo la podyera pao siligulika; popeza ndilo lao lao kosatha.
35 Ndipo mbale wako akasaukira cuma, ndi dzanja lace lisowa; iwe uzimgwiriziza; akhale nawe monga mlendo wakugonera kwanu.
36 Usamambwezetsa phindu, kapena cioniezero; koma uope Mulungu wako; kuti mbale wako akhale nawe.
37 Musamampatsa ndarama zako polira phindu, kapena kumpatsa zakudya kuti aonjezerepo pocibwezera.
38 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakuturutsani m'dziko la Aigupto, kukupatsani dziko la Kanani, kuti ndikhale Mulungu wanu.
39 Ndipo mbale wako akasaukira cuma, ndi kudzigulitsa kwa iwe; usamamgwiritsa nchito monga kapolo;
40 azikhala nawe ngati wolipidwa nchito, ngati munthu wokhala nawe; akutumikire kufikira caka coliza lipenga.
41 Pamenepo azituruka kukucokera, iye ndi ana ace omwe, nabwerere ku mbumba yace; abwerere ku dziko lao lao la makolo ace.
42 Pakuti iwo ndiwo atumiki anga, amene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto; asamawagulitsa monga amagulitsa kapolo.
43 Usamamweruza momzunza; koma uope Mulungu wako.
44 Kunena za kapolo wako wamwamuna, kapena wamkazi amene ukhala nao; azikhala a amitundu akuzungulira inu, kwa iwowa muzigula akapolo amuna ndi akazi.
45 Muwagulenso ana a alendo akukhala mwa inu, a iwowa ndi a mabanja ao akukhala nanu, amene anabadwa m'dziko lanu; ndipo adzakhala anu anu.
46 Ndipo muwayese colowa ca ana anu akudza m'mbuyo, akhale ao ao; muwayese akapolo kosatha; koma za abale anu, ana a Israyeli, musamalamulirana mozunza.
47 Ndipo mlendo wakugonera kwanu akalemera cuma, ndi mbale wako wakukhala naye akasauka, nadzigulitsa kwa mlendo wakugonera kwanu, kapena kwa pfuko la banja la mlendo;
48 atatha kudzigulitsa, aomboledwe; wina wa abale ace amuombole;
49 kapena mbale wa atate wace, kapena mwana wa mbale wa atate wace amuombole, kapena mbale wace ali yense wa banja lace amuombole; kapena akalemera cuma yekha adziombole yekha.
50 Ndipo awerengere amene anamgulayo kuyambira caka adadzigulitsa kwa iye kufikira caka coliza lipenga; ndipo mtengo wace ukhale monga mwa kuwerenga kwa zaka; amuyesere monga masiku a munthu wolipidwa.
51 Zikamtsalira zaka zambiri, monga mwa izi abwezere ndarama zakumuombola zocokera ku ndalama zomgulazo.
52 Ndipo zikamtsalira zaka pang'ono kufikira caka coliza lipenga amwerengere; monga mwa zaka zace abwezere mtengo wace wakumuombola.
53 Akhale naye monga wolipidwa caka ndi caka; asamamlamulira momzunza pamaso pako,
54 Ndipo akapanda kumuombola motero, azituruka caka coliza lipenga, iye ndi ana ace omwe.
55 Pakuti ana a Israyeli ndi atumiki anga; iwo ndiwo atumiki anga amene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
1 Musamadzipangira mafano, kapena kudziutsira mafano osema, kapena coimiritsa, kapena kuika mwala wozokota m'dziko mwanu kuugwadira umene; popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
2 Musunge masabata anga, ndi kucitira ulemu malo anga opatulika; Ine ndine Yehova.
3 Mukamayenda m'malemba anga, ndi kusunga malamulo anga, ndi kuwacita;
4 ndidzakupatsani mvula m'nyengo zace, ndi dziko lidzapereka zipatso zace, ndi mitengo ya m'minda idzabala zipatso zace.
5 Ndipo nyengo yopuntha tirigu idzafikira nyengo yochera mphesa, ndi nyengo yochera mphesa idzafikira nyengo zobzala; ndipo mudzakhuta naco cakudya canu, ndi kukhala m'dziko mwanu okhazikika.
6 Ndipo ndidzapatsa mtendere m'dzikomo, kuti mudzagone pansi, wopanda wina wakukuopsani; ndidzaletsanso zirombo zisakhale m'dzikomo, lupanga lomwe silidzapita m'dziko mwanu.
7 Mudzapitikitsa adani anu, ndipo adzagwa pamaso panu ndi lupanga,
8 Asanu ainu adzapitikitsa zana limodzi, ndi zana limodzi la inu adzapitikitsa zikwi khumi; ndi adani anu adzagwa pamaso panu ndi lupanga.
9 Ndipo ndidzatembenukira kwa inu, ndi kukubalitsani, ndi kukucurukitsani; ndipo ndidzakhazika cipangano canga ndinapangana nanuco.
10 Ndipo mudzadya za sundwe wakale ndi kuturutsa zakale cifukwa ca zatsopano.
11 Ndidzamanga kacisi wanga pakati pa inu, ndipo moyo wanga sudzanyansidwa nanu.
12 Ndipo ndidzayendayenda pakati pa inu, ndi kukhala Mulungu wanu ndi inu mudzakhala anthu anga.
13 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakuturutsani m'dziko la Aigupto, kuti musakhale akapolo ao; ndipo ndinatyola mitengo ya magoli anu, ndi kukuyendetsani coweramuka.
14 Koma mukapanda kundimvera Ine, osacita malamulo awa onse;
15 ndipo mukakaniza malemba anga, ndi moyo wanu ukanyansidwa nao maweruzo anga, kotero kuti simudzacita malamulo anga onse, koma kutyola cipangano canga;
16 ndidzacitira inu icinso; ndidzakuikirani zoopsa, nthendayoondetsayam'cifuwa ndi malungo, zakulanda maso ndi mphamvu, ndi kuzunza moyo; ndipo mudzabzala mbeu zanu cabe, pope za adani anu adzazidya.
17 Ndipt nkhope yanga idzatsutsana nanu kuti adani anu adzakukanthani, ndipt akudana ndi inu adzacita ufumu Pl inu ndipo mudzathawa wopanda wakukulondolani.
18 Ndipo muka panda kundimvera, zingakhale izi ndidzaonjeza kukulangani kasanu nd kawiri cifukwa ca zocimwa zanu.
19 Popeza ndidzatyola mphamvu yam yodzikuza; ndi kusandutsa thambo lanu likhale ngati citsulo ndi dziko lanu ngati mkuwa;
20 ndipo mudzacita nayo mphamvu yanu cabe; ndi nthaka yanu siidzapereka zipatse zace, ndi mitengo ya m'dziko siidzabala zobala zace.
21 Ndipo mukayenda motsutsana nane, osalola kumvera Ine; ndidzakuonjezerani miliri kasanu ndi kawiri, monga mwa zocimwa zanu.
22 Popeza ndidzatumiza cirombo ca kuthengo pakati pa inu, ndipo cidzalanda ana anu, ndi kuononga zoweta zanu nicidzacepetsa inu kuti mukhale pang'ono; ndi njira zanu zidzakhala zakufa.
23 Ndipo mukapanda kulangika nazo ndi kubwera kwa Ine, mukayenda motsutsana ndi Ine;
24 Inenso ndidzayenda motsutsana ndi inu; ndipo ndidzakukanthani Inedi kasanu ndi kawiri cifukwa ca zoipa zanu.
25 Ndipo ndidzadzetsa kwa inu lupanga lakucita cilango ca cipangano; kotero kuti mudzasonkhanidwa m'midzi mwanu; ndipo ndidzatumiza mliri pakati pa inu; ndipo mudzaperekedwa m'manja mwa mdani.
26 Pamene ndityola mcirikizo wanu wa mkate, akazi khumi adzaphika mkate wanu mu mcembo umodzi, nadzabweza mkate wanu ndi kuuyesa; ndipo mudzadya, koma osakhuta.
27 Ndipo mukapanda kundimvera Ine, cingakhale ici, ndi kuyenda motsutsana nane;
28 Ine ndidzayenda nanu motsutsana mwa kukuzazirani, ndi kukulangani Inedi kasanu ndi kawiri cifukwa ca zocimwa zanu.
29 Ndipo mudzadya nyama ya ana anu amuna; inde nyama ya ana anu akazi mudzaidya.
30 Ndipo ndidzaononga malo amsanje anu, ndi kulikha zoimiritsa zanu za dzuwa, ndi kuponya mitembo yanu pa mitembo ya mafano anu; ndi moyo wanga udzanyansidwa nanu.
31 Ndipo ndidzasandutsa midzi yanu bwinja, ndi kupasula malo anu opatulika, wosanunkhiza Ine za pfungo lanu lokoma.
32 Inde, ndidzapasula dzikoli, ndipo adani anu akukhala m'mwemo adzadabwa nako.
33 Ndipo ndidzabalalitsa inu mwa amitundu, ndi kusolola lupanga kukutsatani; ndi dziko lanu lidzakhala lopasuka, ndi midzi yanu idzakhala bwinja.
34 Pamenepo dzikoli lidzakondwera nao masabata ace, masiku onse a kupasuka kwace, pokhala inu m'dziko la adani anu; pamenepo dziko lidzapumula, ndi kukondwera nao masabata ace.
35 Masiku onse a kupasuka kwace lipumula; ndiko mpumulo udalisowa m'masabata anu, pokhala inu pamenepo.
36 Kunena za iwo akutsalira, ndidzalonga kukomoka kumtima kwao m'maiko a adani ao; ndi liu la tsamba lotengeka ndi mphepo lidzawapitikitsa; ndipo adzathawa monga amathawa lupanga; ndipo adzagwa wopanda wakuwalondola.
37 Ndipo adzakhumudwitsana monga pothawa lupanga, wopanda wakuwalondola; ndipo mudzakhala opanda mphamvu yakuima pamaso pa adani anu.
38 Ndipo mudzatayika mwa amitundu, ndi dziko la adani anu lidzakudyani.
39 Ndipo otsala mwa inu adzazunzika m'moyo ndi mphulupulu zao m'maiko a adani anu; ndiponso ndi mphulupulu za makolo ao adzazunzika m'moyo.
40 Pamenepo adzabvomereza mphulupulu zao, ndi mphulupulu za makolo ao, pocita zosakhulupirika pa Ine; ndiponso popeza anayenda motsutsana ndi Ine,
41 Inenso ndinayenda motsutsana nao, ndi kuwatengera ku dziko la adani ao. Ngati tsono mtima wao wosadulidwa udzicepetsa, ndipo abvomereza kulanga kwa mphulupulu zao;
42 pamenepo ndidzakumbukila pangano langa ndi Yakobo; ndiponso pangano langa ndi Isake, ndiponso pangano langa ndi Abrahamu ndidzakumbukila; ndipo ndidzakumbukila dzikoli.
43 Dziko lomwe lidzasiyidwa nao, ndi kukondwera ndi masabata ace, pokhala lopasuka, iwowa palibe; ndipo iwo adzabvomereza kulanga kwa mphulupulu zao; popeza, inde popeza anakaniza maweruzo anga, ndi moyo wao unanyansidwa nao malemba anga.
44 Ndiponso pali icinso: pokhala iwo m'dziko la adani ao sindidzawakaniza, kapena kunyansidwa nao, kuwaononga konse, ndi kutyola pangano langa ndinapangana nao; popeza Ine ndine Yehova Muhmgu wao.
45 Koma cifukwa ca iwo ndidzawakumbukila pangano la makolo ao, amene ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto pamaso pa amitundu, kuti ndikhale Mulungu wao; Ine ndine Yehova.
46 Awa ndi malemba ndi maweruzo ndi malamulo amene Yehova anaika pakati pa iye ndi ana a Israyeli m'phiri la Sinai, ndi dzanja la Mose.
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2 Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Pamene munthu acita cowinda ca padera, anthuwo azikhala a Yehova monga mwa kuyesa kwako.
3 Ukayesa wamwamuna wa zaka makumi awiri kufikira wina wa zaka makumi asanu ndi limodzi, uziwayesera a masekeli makumi asanu a siliva, monga mwa sekeli wa malo opatulika.
4 Koma akakhala wamkazi, umuyesere wa masekeli makumi atatu.
5 Akakhala munthu wa zaka zisanu kufikira wina wa zaka makumi awiri uwayesere, wamwamuna wa masekeli makumi awiri, ndi wamkazi wa masekeli khumi.
6 Akakhala mwana wa mwezi umodzi kufikira zaka zisanu, uziwayesera wamwamuna wa masekeli asanu a siliva, ndi wamkazi wa masekeli atatu a siliva.
7 Akakhala munthu wa zaka makumi asanu ndi limodzi ndi mphambu, akakhala wamwamuna, umuyesere wa masekeli khumi ndi asanu, akakhala wamkazi wa masekeli khumi.
8 Koma cuma cace cikapanda kufikira kuyesa kwako, amuike pamaso pa wansembe, kuti wansembeyo amuyese; ndipo wansembeyo amuyese, monga akhoza iye amene anawinda.
9 Ndipo cikakhala ca nyama imene anthu amabwera nayo ikhale copereka ca Yehova, zonse zotere munthu akazipereka kwa Yehova zikhale zopatulika.
10 Asaisinthe, yokoma m'malo mwa yoipa, kapena yoipa m'malo mwa yokoma; ndipo akasinthadi nyama m'malo mwa inzace, pamenepo iyo ndi yosinthikayo zikhale zopatulika.
11 Ndipo cikakhala ca nyama yodetsa, imene sabwera nayo ikhale copereka ca Yehova, aike nyamayi pamaso pa wansembe;
12 ndipo wansembeyo aiyese mtengo wace, ingakhale yokoma kapena yoipa; monga uiyesa wansembewe, momwemo.
13 Ndipo akaiombola ndithu, pamenepo aonjezepo limodzi la magawo asanu la mtengo wace.
14 Munthu akapatula nyumba yace ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe aziiyesa mtengo wace, ingakhale yokoma kapena yoipa; monga wansembeyo aiyesa, ikhale momwemo.
15 Ndipo iye wakuipatula akaombola nyumba yace, aonjezepo limodzi la magawo asanu la ndalama za kuyesa kwako, ndipo idzakhala yace.
16 Munthu akapatulirako Yehova munda wace wace, uziuyesa monga mwa mbeu zace zikakhala; homeri wa barie uuyese wa masekeli makumi asanu a siliva.
17 Akapatula munda wace kuyambira caka coliza lipenga, mundawo ukhale monga momwe unauyesera.
18 Akaupatula munda wace citapita caka coliza lipenga, wansembe azimwerengera ndalama monga mwa zaka zotsalira kufikira caka coliza lipenga, nazicepsako pa kuyesa kwako.
19 Ndipo wakupacula mundayo akauomboladi, aonjezeko limodzi la magawo asanu la ndalama za kuyesa kwako, ndipo uzikhalitsa wace.
20 Koma akapanda kuombola mundawo, kapena atagulitsa mundawo kwa munthu wina, suomboledwanso;
21 koma poturuka m'caka coliza lipenga, mundawo ukhale wopatulikira Yehova, ngati munda woperekedwa ciperekere kwa Mulungu; ukhale wace wace wa wansembe.
22 Ndipo akapatulira Yehova munda woti adaugula, wosati wogawako ku munda wace wace;
23 pamenepo wansembeyo amwerengere mtengo wace wa kuyesa kwako kufikira caka coliza lipenga; ndipo apereke kuyesa kwako tsiku lomwelo, cikhale cinthu copatulikira Yehova,
24 Caka coliza lipenga mundawo ubwerere kwa iye amene adaugulitsa, kwa iye amene dzikoli ndi lace lace.
25 Ndipo kuyesa kwako konse kukhale monga mwa sekeli wa malo opatulika; sekeli ndi magera makumi awiri.
26 Komatu woyamba kubadwa mwa nyama akhale wobadwa woyamba wa Yehova, munthu asampatule; ingakhale ng'ombe ingakhale nkhosa, ndiye wa Yehova.
27 Koma akakhala wa nyama zodetsa, azimuombola monga mwa kuyesa kwako, naonjezepo limodzi la magawo asanu la mtengo wace; ndipo akapanda kumuombola, amgulitse monga mwa kuyesa kwako.
28 Koma asacigulitse kapena kuciombola cinthu coperekedwa ciperekere kwa Mulungu, cimene munthu acipereka ciperekere kwa: Yehova, cotengako ku zonse ali nazo, ngakhale munthu, kapena nyama, kapena munda wace wace; ciri conse coperekedwa ciperekere kwa Mulungu neopatulikitsa.
29 Asamuombole munthu woperekedwa ciperekere kwa Mulungu; amuphe ndithu.
30 Limodzi mwa magawo khumi la zonse m'dziko, la mbeu zace za dziko, la zipatso za mtengo, ndilo la Yehova; likhale lopatulikira Yehova.
31 Koma munthu akaombolatu kanthu ka limodzi la magawo khumiwo aonjezeko limodzi la magawo asanu.
32 Ndipo limodzi la magawo khumi lonse la ng'ombe, kapena la nkhosa, kapena la mbuzi, ziri zonse zimapita pansi pa ndodo, limodzi la magawo khumi likhale lopatulikira Yehova.
33 Asafunse ngati yabwino kapena yoipa, kapena kuisintha; koma akaisinthatu, pamenepo iyo ndi yosinthikayo zikhale zopatulika zonse ziwiri; asamaiombola.
34 Awa ndi malamulo, amene Yehova anauza Mose, awauze ana a Israyeli, m'phiri la Sinai.