1

1 ADAMU, Seti, Enosi,

2 Kenani, Mahalaheli, Yaredi,

3 Enoki, Metusela, Lameki,

4 Nowa, Semu, Hamu, ndi Yafeti.

5 Ana a Yafeti: Gomeri, ndi Magogi, ndi Madai, ndi Yavani, ndi Tubala, ndi Meseki, ndi Tirasi.

6 Ndi ana a Gomeri: Asikenazi, Difati, ndi Togarima.

7 Ndi ana a Yavani: Elisa, ndi Tarisisa, Kitimu, ndi Rodanimu.

8 Ana a Hamu: Kusi, ndi Mizraimu, Puti, ndi Kanani.

9 Ndi ana a Kusi: Seba, ndi Havila, ndi Sabita, ndi Rama, ndi Sabteka. Ndi ana a Rama: Seba, ndi Dedani.

10 Ndi Kusi anabala Nimmdi; iye anayamba kukhala wamphamvu pa dziko.

11 Ndi Mizraimu anabala Aludi, ndi Aanami, ndi Alehabi, ndi Anaftuki,

12 ndi Apatrusi, ndi Akasluki, (kumene anafuma Afilisti), ndi Akafitori.

13 Ndi Kanani anabala Zidoni mwana wace woyamba, ndi Heti,

14 ndi Ayebusi, ndi Aamori, ndi Agirigasi,

15 ndi Ahivi, ndi Aariki, ndi Asini,

16 ndi Aarivadi, ndi Azemari, ndi Ahamati.

17 Ana a Semu: Elamu, ndi Asuri, ndi Aripakisadi, ndi Ludi, ndi Aramu, ndi Uzi, ndi Huli, ndi Geteri, ndi Meseki.

18 Ndi Aripakisadi anabala Sela; ndi Sela anabala Eberi.

19 Ndi Eberi anabala ana amuna awiri, dzina la winayo ndiye Pelegi, popeza masiku ace dziko linagawanika; ndi dzina la mbale wace ndiye Yokitani.

20 Ndipo Yokitani anabala Almodadi, ndi Selefi, ndi Hazaramaveti, ndi Yera;

21 ndi Hadoramu, ndi Uzali, ndi Dikila;

22 ndi Ebala, ndi Abimaele, ndi Seba,

23 ndi Ofiri, ndi Havila, ndi Yobabi. Awa onse ndiwo ana a Yokitani.

24 Semu, Aripakisadi, Sela;

25 Eberi, Pelegi, Reu,

26 Serugi, Nahori, Tera;

27 Abramu, (ndiye Abrahamu).

28 Ana a Abrahamu: Isake, ndi Ismayeli.

29 Mibadwo yao ndi awa; woyamba wa Ismayeli Nebayoti; ndi Kedara ndi Adibeli, ndi Mibisamu,

30 Misma, ndi Duma Masa,

31 Hadada, ndi Tema, Nafisi, ndi Kedema. Awa ndi ana a Ismayeli.

32 Ndi ana a Ketura mkazi wamng'ono wa Abrahamu anabala Zimiramu, ndi Yokisani, ndi Medani, ndi Midyani, ndi Isibaki, ndi Sua. Ndi ana a Yokisani: Seba, ndi Dedani.

33 Ndi ana a Midyani: Efa, ndi Eferi, ndi Hanoki, ndi Abida, ndi Elidaa. Awa onse ndiwo ana a Ketura.

34 Ndipo Abrahamu anabala Isake. Ana a Isake: Esau, ndi Israyeli.

35 Ana a Esau: Elifazi, Reueli, ndi Yeuzi, ndi Yolamu, ndi Kora.

36 Ana a Elifazi: Teani, ndi Omara, Zefi, ndi Gatamu, Kenazi, ndi Timna, ndi Amaleki.

37 Ana a Reueli: Nahati, Zera, Sama, ndi Miza.

38 Ndi ana a Seiri: Lotani, ndi Sobala, ndi Zibeoni, ndi Ana, ndi Disoni, ndi Ezeri, ndi Disani.

39 Ndi ana a Lotani: Hori, ndi Homamu; ndipo Timna ndiye mlongo wace wa Lotani.

40 Ana a Sobala: Abiani, ndi Manahati, ndi Ebala, Sefi, ndi Oramu. Ndi ana a Zibeoni: Aiya ndi Ana.

41 Mwana wa Ana: Disoni. Ndi ana a Disoni: Hamirani, ndi Esibani, ndi Itrani, ndi Kerani.

42 Ana a Ezeri: Bilani, ndi Zavani, ndi Yakani. Ana a Disani: Uzi, ndi Arani.

43 Mafumu tsono akucita ufumu m'dziko la Edomu, pakalibe mfumu wakucita ufumu pa ana a Israyeli, ndiwo Bela mwana wa Beori; ndi dzina la mudzi wace ndilo Dinaba.

44 Ndipo anafa Bela; ndi Yobabi mwana wa Zera wa ku Bozra anakhala mfumu m'malo mwace.

45 Namwalira Yobabi; ndi Husamu wa ku dziko la Atemani anakhala mfumu m'malo mwace.

46 Namwalira Husamu; ndi Hadada mwana wa Bedadi, amene anakantha Midyani ku thengo la Moabu, anakhala mfumu m'malo mwace; ndi dzina la mudzi wace ndi Aviti.

47 Namwalira Hadada; ndi Samla wa ku Masereka anakhala mfumu m'malo mwace.

48 Namwalira Samla: ndi Sauli wa ku Rehoboti ku nyanja anakhala mfumu m'malo mwace.

49 Namwalira Sauli; ndi Baalahanani mwana wa Akiboro anakhala mfumu m'malo mwace.

50 Namwalira Baalahanani; ndi Hadada anakhala mfumu m'malo mwace; ndipo dzina la mudzi wace ndi Pai; ndi dzina la mkazi wace ndiye Mehetabele mwana wamkazi wa Matradi mwana wamkazi wa Mezahabu.

51 Namwalira Hadada. Ndipo mafumu a Edomu ndiwo mfumu Timna, mfumu Aliya, mfumu Yeteti;

52 mfumu Oholibama, mfumu Bla, mfumu Pimoni;

53 mfumu Kenazi, mfumu Temani, mfumu Mizibara;

54 mfumu Magadieli, mfumu Iramu. Awa ndi mafumu a Edomu.

2

1 Ana a Israyeli ndi awa: Rubeni, Simeoni, Levi, ndi Yuda, Isakara, ndi Zebuluni,

2 Dani, Yosefe, ndi Benjamini, Nafitali, Gadi, ndi Aseri.

3 Ana a Yuda ndiwo Eri, ndi Onani, ndi Sela; Batisua Mkanani anambalira atatu amenewa. Koma Eri mwana woyamba wa Yuda anali woipa pamaso pa Yehova, ndi iye anamupha.

4 Ndi Tamari mpongozi wace anambalira Perezi ndi Zera. Ana amuna onse a Yuda ndiwo asanu.

5 Ana a Perezi: Hezironi, ndi Hamuli.

6 Ndi ana a Zera: Zimri, ndi Etani, ndi Hemani, ndi Kalikoli, ndi Dara; onse pamodzi ndi asanu.

7 Ndi ana a Karmi: Akari wobvuta Israyeliyo, amene analakwira coperekedwa ciperekereco.

8 Ndi mwana wa Etani: Azariya.

9 Ndi ana a Hezironi anambadwirawo: Yerameli, ndi Ramu, ndi Kelubai.

10 Ndi Ramu anabala Aminadabu; ndi Aminadabu anabala Nasoni kalonga wa ana a Yuda;

11 ndi Nasoni anabala Salima, ndi Salima anabala Boazi,

12 ndi Boazi anabala Obedi, ndi Obedi anabala Jese,

13 ndi Jese anabala mwana wace wamwamuna woyamba Eliabu, ndi Abinadabu waciwiri, ndi Simeya wacitatu,

14 Netaneli wacinai, Radai wacisanu,

15 Ozemu wacisanu ndi cimodzi, Davide wacisanu ndi ciwiri;

16 ndi alongo ao ndiwo Zeruya ndi Abigaili. Ndi ana a Zeruya: Abisai ndi Yoabu, ndi Asaheli; atatu.

17 Ndi Abigaili anabala Amasa; ndi atate wa Amasa ndiye Yeteri M-ismayeli.

18 Ndi Kalebi mwana wa Hezroni anabala ana ndi Azuba mkazi wace, ndi Yerioti; ndipo ana ace ndiwo Yeseri, ndi Sobabu, ndi Aridoni.

19 Namwalira Azuba, ndi Kalebi anadzitengera Efrati, amene anambalira Huri.

20 Ndi Huri anabala Uri, ndi Uri anabala Bezaleli.

21 Ndipo pambuyo pace Hezroni analowa kwa mwana wamkazi wa Makiri atate wa Gileadi, amene anamtenga akhale mkazi wace, pokhala wa zaka makumi asanu ndi Gmodzi mwamunayo; ndipo mkaziyo anambalira Segubu.

22 Ndi Segubu anabala Yairi, amene anali nayo midzi makumi awiri mphambu itatu m'dziko la Gileadi.

23 Ndi Gesuri ndi Aramu analanda midzi ya Yairi, pamodzi ndi Kenati ndi miraga yace; ndiyo midzi makumi asanu ndi limodzi. Iwo onse ndiwo ana a Makiri atate wa Gileadi.

24 Ndipo atafa Hezroni m'Kalebi-Efrata, Abiya mkazi wa Hezroni anambalira Asini atate wa Tekoa.

25 Ndi ana a Yerameli mwana woyamba wa Hezroni ndiwo: woyamba Ramu, ndi Buna, ndi Oreni, ndi Ozemu, ndi Ahiya.

26 Ndipo Yerameli anali naye mkazi wina dzina lace ndiye Atara, ndiye mace wa Onamu.

27 Ndipo ana a Ramu mwana woyamba wa Yerameli ndiwo Maazi, ndi Yamini, ndi Ekeri.

28 Ndi ana a Onamu ndiwo Samai, ndi Yada; ndi ana a Samai: Nadabu, ndi Abisuri.

29 Ndipo dzina la mkazi wa Abisuri ndiye Abihaili; ndipo anambalira Abani, ndi Molidi.

30 Ndi ana a Nadabu: Seledi ndi Apaimu; koma Seledi anamwalira wopanda ana.

31 Ndi mwana wa Apaimu: lsi. Ndi mwana wa lsi: Sesani. Ndi mwana wa Sesani: Alai.

32 Ndi ana a Yada mbale wa Samai: Yeteri, ndi Yonatani; namwalira: Yeteri wopanda ana.

33 Ndi ana a, Yonatani: Peleti, ndi Zaza. Ndiwo ana a Yerameli.

34 Ndipo Sesani analibe ana amuna, koma ana akazi. Ndi Sesani anali naye mnyamata M-aigupto dzina lace ndiye Yara.

35 Ndipo Sesani anampatsa Yara mnyamata wace mwana wace wamkazi akhale mkazi wace, ndipo anambalira Atai.

36 Ndipo Atai anabala Natani, ndi Natani anabala Zabadi,

37 ndi Zabadi anabala Efilali, ndi Efilali anabala Obedi,

38 ndi Obedi anabala Yehu, ndi Yehu anabala Azariya,

39 ndi Azariya anabala Helezi, ndi Helezi anabala Eleasa,

40 ndi Eleasa anabala Sismai, ndi Sismai anabala Salumu,

41 ndi Salumu anabala Yekamiya, ndi Yekamiya anabala Elisama.

42 Ndi ana a Kalebi mbale wa Yerameli ndiwo Mesa mwana wace woyamba, ndiye atate wa Zifi; ndi ana a Maresa atate wa Hebroni.

43 Ndi ana a Hebroni: Kora, ndi Tapuwa, ndi Rekemu, ndi Sema.

44 Ndi Sema anabala Rahamu atate wa Yorikeamu, ndi Rekemu anabala Samai.

45 Ndi mwana wa Samai ndiye Maoni; ndipo Maoni ndiye atate wa Betizuri.

46 Ndi Efa mkazi wamng'ono wa Kalebi anabala Harani, ndi Moza, ndi Gazezi; ndi Harani anabala Gazezi.

47 Ndi ana a Yadai: Regemu, ndi Yotamu, ndi Gesam, ndi Peleti, ndi Efa, ndi Safa.

48 Maka mkazi wamng'ono wa Kalebi anabala Seberi, ndi Tirana.

49 Iyeyu anabalanso Safa atate wa Madimana, Seva atate wa Makibena, ndi atate wa Gibeya; ndi mwana wamkazi wa Kalebi ndiye Akisa.

50 Ana a Kalebi ndi awa: mwana wa Huri, mwana woyamba wa Efrata, Sobali atate wa Kiriate Yearimu.

51 Salma atate wa Betelehemu, Harefi atate wa Betigaderi.

52 Ndipo Sobali atate wa Kiriati-Yearimu anali ndi ana: Haroe, ndi Hazi Hamenukoti.

53 Ndi mabanja a Kiriati-Yearimu: Aitiri, ndi Aputi, ndi Asumati, ndi Amisrai; Aforati ndi Aestaoli anafuma kwa iwowa.

54 Ana a Salma: Betelehemu, ndi Anetofati, Atroti Beti Yoabu, ndi Hazi Hamanahati, ndi Azori.

55 Ndi mabanja a alembi okhala ku Yabezi: Atirati, Asimeati, Asukati. Iwo ndiwo Akeni ofuma ku Hamati, kholo la nyumba ya Rekabu.

3

1 Ana Davide tsono ombadwira ku Hebroni: woyamba a Amnoni wa Ahinoamu wa ku Yezreeli, waciwiri Danieli wa Abigaili wa ku Karimeli,

2 wacitatu Abisalomu mwana wa Maaka mwana wamkazi wa Talimai mfumu ya Gesuri, wacinai Adoniya mwana wa Hagiti,

3 wacisanu Sefatiya wa Abitali, wacisanu ndi cimodzi Itreamu wa mkazi wace Egila,

4 Anambadwira asanu ndi mmodzi m'Hebroni; ndi pomwepo anakhala mfumu zaka zisanu ndi ziwiri, ndi miyezi isanu ndi iwiri; ndi m'Yerusalemu anakhala mfumu zaka makumi atatu mphambu zitatu.

5 Ndipo ombadwira m'Yerusalemu ndi awa: Simeya, ndi Sobabu, ndi Natani, ndi Solomo, anai a Batisuwa mwana wamkazi wa Amieli;

6 ndi Ibara, ndi Elisama, ndi Elifeleti,

7 ndi Noga, ndi Nefegi, ndi Yafiya,

8 ndi Elisama, ndi Eliada, ndi Elifeleti, asanu ndi anai.

9 Onsewa ndiwo ana a Davide, pamodzi ndi ana a akazi ang'ono; ndipo Tamara ndiye mlongo wao.

10 Ndipo mwana wa Solomo ndiye Rehabiamu, Abiya mwana wace, Asa mwana wace, Yeo hosafati mwana wace,

11 Yoramu mwana wace, Ahaziya mwana wace, Yoasi mwana wace,

12 Amaziya mwana wace, Azariya mwana wace, Yotamu mwana wace,

13 Ahazi mwana wace, Hezekiya mwana wace, Manase mwana wace,

14 Amoni mwana wace, Yosiya mwana wace.

15 Ndi ana a Yosiya: woyamba Yohanana, waciwiri Yehoyakimu, wacitatu Zedekiya, wacinai Salumu.

16 Ndi ana a Yehoyakimu: Yekoniya mwana wace, Zedekiya mwana wace.

17 Ndi mwana wa Yekoniya: Asiri, Sealitiyeli mwana wace,

18 ndi Malikiramu, ndi Pedaya, ndi Senazara, Yekamiya, Hosama, Nedabiya.

19 Ndi ana a Pedaya: Zerubabeli, ndi Simei; ndi ana a Zerubabeli: Mesulamu, ndi Hananiya; ndipo Selomiti ndiye mlongo wao,

20 ndi Hasuba, ndi Oheli, ndi Berekiya, ndi Hasadiya, ndi Yusabi-hesedi; asanu.

21 Ndi ana a Hananiya: Pelatiya, ndi Yesaya, ana a Refaya, ana a Arinani, ana a Obadiya, ana a Sekaniya.

22 Ndi mwana wa Sekaniya: Semaya; ndi ana a Semaya: Hatusi, ndi Igali, ndi Bariya, ndi Neariya, ndi Safati; asanu ndi mmodzi.

23 Ndi ana a Neariya: Eliunai, ndi Hizikiya, ndi Azrikamu, atatu.

24 Ndi ana a Eliunai: Hodavia, ndi Eliasibu, ndi Pelaya, ndi Akubu, ndi Yohanana, ndi Delaya, ndi Anani, asanu ndi awiri.

4

1 Ana a Yuda: Perezi, Hezroni, ndi Karmi, ndi Huri, ndi Sobala.

2 Ndipo Reaya mwana wa Sobala anabala Yahati; ndi Yahati anabala Ahumai, ndi Lahadi. Iwo ndiwo mabanja a Azorati.

3 Iwo ndiwo a atate wa Etamu: Yezreeli, ndi Isma, ndi Idibasi; ndipo dzina la mlongo wao ndiye Hazeleleponi,

4 ndi Penueli atate wa Gedoro, ndi Ezeri atate wa Husa. Awa ndi ana a Huri woyamba wa Efrata atate wa Betelehemu.

5 Ndipo Asuri atate wa Tekowa anali nao akazi awiri: Hela, ndi Naara.

6 Ndi Naara anambalira Ahuzamu, ndi Heferi, ndi Temeni, ndi Hahastario Iwo ndiwo ana a Naara.

7 Ndi ana a Hela ndiwo Zereti, lzara, ndi Etinani.

8 Ndipo Hakozi anabala Anubu, ndi Zobeba, ndi mabanja a Ahareli mwana wa Harumu.

9 Ndipo Yabezi analemekezedwa koposa abale ace; ndi mace anamucha dzina lace Yabezi, ndi kuti, Popeza ndambala mwaululu.

10 Ndipo Yabezi anaitana kwa Mulungu wa Israyeli, ndi kuti, Mundidalitse ndithu, ndi kukulitsa malire anga; ndi dzanja lanu likhale ndi ine, nimundisunge, kuti coipa cisandibvute. Ndipo Mulungu anafikitsa copempha iye.

11 Ndipo Kelubu mbale wa Sua anabala Mehiri, ndiye atate wa Esitoni.

12 Ndi Esitoni anabala Betirafa, ndi Paseya, ndi Tehina atate wa Irinahasi. Awa ndi anthu a Reka.

13 Ndi ana a Kenazi: Otiniyeli, ndi Seraya; ndi mwana wa Otmiyeh: Hatati.

14 Ndipo Meonotai anabala Ofra; ndi Seraya anabala Yoabu atate wa Geharasimu; popeza iwo ndiwo amisiri.

15 Ndi ana a Kalebi mwana wa Yefune: Iru, Ela, ndi Naamu; ndi ana a Ela, ndi Kenazi.

16 Ndi ana a Yehaleleli: Ziti, ndi Zifa, Tiriya, ndi Asareli.

17 Ndi ana a Ezra: Yeteri, ndi Meredi, ndi Eferi, ndi Yaloni; ndipo anabala Miriamu, ndi Samai, ndi Isba atate wa Esitemowa.

18 Ndi mkazi wace Myuda anabala Yeredi atate wa Gedoro, ndi Heberi atate wa Soko, ndi Yekutiyeli atate wa Zanowa. Ndipo awa ndi ana a Bitiya mwana wamkazi wa Farao, amene Meredi anamtenga.

19 Ndi ana a mkazi wa Hodiya, mlongo wace wa Nahamu, ndiwo atate a Kula Mgarimi ndi Esitemowa Mmaaka.

20 Ndi ana a Simoni; Amnoni, ndi Rina, Benehanana, ndi Tiloni. Ndi ana a lsi: Zoheti, ndi Benzoheti.

21 Ana a Sela mwana wa Yuda: Eri atate wa Leka, ndi Laada atate wa Maresa, ndi mabanja a nyumba ya iwo oomba bafuta wa thonje losansitsa a nyumba ya Asibeya,

22 ndi Yokimu, ndi amuna a Kozeba, ndi Yoasi, ndi Sarafa wolamulira m'Moabu, ndi Yasubilehemu; koma mau awa ndiwo a kale lomwe.

23 Iwo ndiwo oumba mbiya, ndi okhala m'Netaimu, ndi m'Gedera; anakhala komweko ndi mfumu m'nchito yace.

24 Ana a Simeoni: Nemueli, ndi Yamini, Yaribi, Zera, Sauli,

25 Salumu mwana wace, Mibsamu mwana wace, Misma mwana wace.

26 Ndi ana a Misma: Hamueli mwana wace, Zakuri mwana wace, Simei mwana wace.

27 Ndipo Simei anali nao ana amuna khumi mphambu asanu ndi mmodzi, ndi ana akazi asanu ndi mmodzi; koma abale ace analibe ana ambiri, ndi banja lao lonse silinacurukitsa ngati ana a Yuda.

28 Ndipo anakhala ku Beereseba, ndi Molada, ndi Hazarasuala,

29 ndi ku Bila, ndi ku Ezemu, ndi ku Toladi,

30 ndi ku Betueli, ndi ku Horima, ndi ku Zikilaga,

31 ndi ku Betimarikaboti, ndi ku Hazarasusimu, ndi ku Betibiri, ndi ku Saraimu. Iyi ndi midzi yao, mpaka ufumu wa Davide, pamodzi ndi miraga yao.

32 Etamu, ndi Aini, Rimoni, ndi Tokeni, ndi Asani, midzi isanu;

33 ndi miraga yao yonse pozungulira pace pa midzi yomweyi, mpaka Baala. Apo ndi pokhala pao ndipo ali nao mawerengedwe a maina ao.

34 Ndi Mesobabu, ndi Yamleki, ndi Yosa mwana wa Amaziya,

35 ndi Yoeli, ndi Yehu mwana wa Yosibiya, mwana wa Seraya, mwana wa Asieli;

36 ndi Eliunai, ndi Yaakoba, ndi Yesohaya, ndi Asaya, ndi Adieli, ndi Yesimieli, ndi Benaya,

37 ndi Ziza mwana wa Sifi, mwana wa Aloni, mwana wa Yedaya, mwana wa Simri, mwana wa Semaya;

38 awa ochedwa maina ndiwo akalonga m'mabanja ao, ndi nyumba za makolo ao zinacuruka kwambiri.

39 Ndipo anamuka mpaka polowera ku Gedoro kum'mawa kwa cigwa, kufunafuna podyetsa zoweta zao.

40 Ndipo anapeza podyetsa ponenepetsa ndi pabwino, ndipo dzikoli ndi lacitando ndi lndikha ndi losungikamo, pakuti okhalako kale ndiwo a Hamu.

41 Iwo tsono olembedwa maina anadza masiku a Hezekiya mfumu ya Yuda, nakantha mahema ao ndi zokhalamo zao, naziononga konse mpaka lero, nakhala m'malo mwao; popeza panali podyetsa zoweta zao pamenepo.

42 Ndipo ena a iwowa a ana a Simeoni, amuna mazana asanu, anamka ku phiri la Seiri; akuwatsogolera ndiwo Pelatiya, ndi Neariya, ndi Refaya, ndi Uzieli; ana a lsi.

43 Nakantha otsala a Aamaleki adapulumukawo, nakhala komweko mpaka lero lino.

5

1 Ndipo ana a Rubeni mwana woyamba wa Israyeli, (pakuti ndiye mwana woyamba; koma popeza anaipsa kama wa atate wace ukulu wace unapatsidwa kwa ana a Yosefe mwana wa Israyeli, koma m'buku la cibadwidwe asayesedwe monga mwa ukulu wace.

2 Pakuti Yuda anakula mphamvu mwa abale ace, ndi mtsogoleri anafuma kwa iyeyu, koma ukulu ngwa Yosefe);

3 ana a Rubeni mwana woyamba wa Israyeli: Hanoki, ndi Palu, Hezroni, ndi Karmi.

4 Ana a Yoeli: Semaya mwana wace, Gogi mwana wace, Simei mwana wace,

5 Mika mwana wace, Reaya mwana wace, Baala mwana wace,

6 Beera mwana wace, amene Tigilati Pilesere wa ku Asuri anamtenga ndende; ndiye kalonga wa Arubeni.

7 Ndi abale ace monga mwa mabanja ao, powerenga cibadwidwe ca mibadwo yao: akuru ndiwo Yeyeli, ndi Zekariya,

8 ndi Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yoeli, wokhala ku Aroeri, ndi kufikira ku Nebo ndi Baala-meoni;

9 ndi kum'mawa anakhala mpaka polowera kucipululu kuyambira mtsinje wa Firate; pakuti zoweta zao zinacuruka m'dziko la Gileadi.

10 Ndipo masiku a Sauli anagwirana nkhondo ndi Ahagiri, amene adagwa ndi dzanja lao; ndipo anakhala m'mahema mwao kum'mawa konse kwa Gileadi.

11 Ndi ana a Gadi anakhala pandunji pao m'dziko la Basana mpaka Saleka:

12 Yoeli mkuru wao, ndi Safamu waciwiri, ndi Yanai, ndi Safati m'Basana;

13 ndi abale ao a; nyumba za makolo ao: Mikaeli, ndi Mesulamu, ndi Seba, ndi Yorai, ndi Yakani, ndi Ziya, ndi Eberi; asanu ndi awiri.

14 Awa ndi ana a Abihaili, mwana wa Huri, mwana wa Yarowa, mwana wa Gileadi, mwana wa Mikaeli, mwana wa Yesisai, mwana wa Yado, mwana wa Buzi,

15 Ahi mwana wa Abdieli, mwana wa Guni, ndiye mkulu wa nyumba za makolo ao.

16 Ndipo anakhala m'Gileadi m'Basana, ndi m'midzi yace, ndi podyetsa pace ponse pa Saroni, mpaka malire ao.

17 Onsewo anawerengedwa monga mwa mabuku a cibadwidwe cao, masiku a Yotamu mfumu ya Yuda, ndi m'masiku a Yerobiamu mfumu ya Israyeli.

18 Ana a Rubeni, ndi a Gadi, ndi limodzi la magawo awiri a pfuko la Manase, ngwazi, amuna akugwira cikopa ndi lupanga, ndi kuponya mibvi, ozerewera nkhondo, ndiwo zikwi makumi anai mphambu zinai mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu ndi limodzi akuturuka kunkhondo.

19 Ndipo anagwirana nkhondo ndi Ahagari, ndi Yet uri, ndi Nafisi, ndi Nodabu.

20 Ndipo anathandizidwa polimbana nao; ndi Ahagari anaperekedwa m'dzanja lao, ndi onse anali nao; pakuti anapfuulira kwa Mulungu pomenyana nao, ndipo anapembedzeka nao, popeza anamkhulupirira iye.

21 Ndipo analanda zoweta zao, ngamila zao zikwi makumi asanu, ndi nkhosa zikwi mazana awiri ndi makumi asanu, ndi aburu zikwi ziwiri, ndi amuna zikwi zana limodzi.

22 Pakuti adagwa, nafa ambiri, popeza nkhondoyi nja Mulungu. Ndipo anakhala m'malo mwao mpaka anatengedwa ndende.

23 Ndi ana a limodzi la magawo awiri a pfuko la Manase anakhala m'dziko; anacuruka kuyambira Basana kufikira Baala Herimoni, ndi Seniri, ndi phiri la Herimoni.

24 Ndipo akuru a nyumba za makolo ao ndi awa: Eferi, ndi lsi, ndi Elieli, ndi Azrieli, ndi Yeremiya, ndi Hodaviya, ndi Yadieli, anthu amphamvu ndithu, anthu omveka, akulu a nyumba za makolo ao.

25 Koma analakwira Mulungu wa makolo ao, nacita cigololo, ndi kutsata milungu ya mitundu ya anthu a m'dziko, amene Mulungu adaononga pamaso pao.

26 Ndipo Mulungu wa Israyeli anautsa mzimu wa Puli mfumu ya Asuri, ndi mzimu wa Tigilati Pilesere mfumu ya Asuri, ndiye anawatenga ndende; ndiwo Arubeni, ndi Agadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati, nafika nao ku Hala, ndi Habori, ndi Hara ndi ku mtsinje wa Gozani, mpaka lero lino.

6

1 Ana a Levi: Gerisomu, Kohati, ndi Merari.

2 Ndi ana a Kohati: Amramu, Izara, ndi Hebroni, ndi Uzieli.

3 Ndi ana a Amramu: Aroni, ndi Mose, ndi Miriamu. Ndi ana a Aroni: Nadabu, ndi Abihu, Eleazara, ndi Itamara.

4 Eleazara anabala Pinehasi, Pinehasi anabala Abisua,

5 ndi Abisua anabala Buki, ndi Buki anabala Uzi,

6 ndi Uzi anabala Zerahiya, ndi Zerahiya anabala Merayoti,

7 Merayoti anabala Amariya, ndi Amariya anabala Ahitubu,

8 ndi Ahitubu anabala Zadoki, ndi Zadoki anabala Ahimaazi,

9 ndi Ahimaazi anabala Azariya, ndi Azariya anabala Yohanani,

10 ndi Yohanani anabala Azariya (ndiye amene anacita nchito ya nsembe m'nyumba anaimanga Solomo m'Yerusalemu),

11 ndi Azariya anabala Amariya, ndi Amariya anabala Ahitubu,

12 ndi Ahitubu anabala Zadoki, ndi Zadoki anabala Salumu,

13 ndi Salumu anabala Hilikiya, ndi Hilikiya anabala Azariya,

14 ndi Azariya anabala Seraya, ndi Seraya anabala Yehozadaki,

15 ndi Yehozadaki analowa undende muja Yehova anatenga ndende Yuda ndi Yerusalemu ndi dzanja la Nebukadinezara.

16 Ana a Levi: Gerisomu, Kohati ndi Merari.

17 Ndipo maina a ana a Gerisomu ndi awa: Libni, ndi Simei.

18 Ndipo ana a Kohati ndiwo Amramu, ndi lzara, ndi Hebroni, ndi Uzieli.

19 Ana a Merari: Mali ndi Musi. Ndi mabanja a Alevi monga mwa nyumba za makolo ao ndi awa.

20 Wa Gerisomu: Libni mwana wace, Yahati mwana wace, Zina mwana wace,

21 Yowa mwana wace, Ido mwana wace, Zera mwana wace, Yeaterai mwana wace.

22 Ana a Kohati: Aminadabu mwana wace, Kora mwana wace, Asiri mwana wace,

23 Elikana mwana wace, ndi Ebiasafu mwana wace, ndi Asiri mwana wace,

24 Tahati mwana wace, Urieli mwana ware, Uziya mwana wace, ndi Sauli mwana wace.

25 Ndi ana a Elikana: Amasai, ndi Ahimoti.

26 Elikana: ana a Elikana Zofai mwana wace, ndi Nahati mwana wace,

27 Eliabu mwana wace, Yerohamu mwana wace, Elikana mwana wace.

28 Ndi ana a Samueli: woyamba Yoeli, ndi waciwiri Abiya.

29 Ana a Merari: Mali, Libni mwana wace, Simei mwana wace, Uza mwana wace,

30 Simeya mwana wace, Hagiya mwana wace, Asaya mwana wace.

31 Ndipo iwo aja Davide anawaimika a udindo wa nyimbo m'nyumba ya Yehova, litafikira kupumula likasalo, ndi awa.

32 Ndipo anatumikira ndi kuyimba pakhomo pa kacisi wa cihema cokomanako mpaka Solomo adamanga nyumba ya Yehova m'Yerusalemu, naimirira m'utumiki wao monga mwa malongosoledwe ao.

33 Ndipo oimirirawo, ndi ana ao, ndi awa: a ana a Akohati, Hemani woyimbayo, mwana wa Yoeli, mwana wa Samueli,

34 mwana wa Elikana, mwana wa Yerohamu, mwana wa Elieli, mwana wa Towa,

35 mwana wa Zufi, mwana wa Elikana, mwana wa Mahati, mwana wa Amasai,

36 mwana wa Elikana, mwana wa Yoeli, mwana wa Azariya, mwana wa Zefaniya,

37 mwana wa Tahati, mwana wa Asiri, mwana wa Abiasafu, mwana wa Kora,

38 mwana wa Izara, mwana wa Kohati, mwana wa Levi, mwana wa Israyeli.

39 Ndi mbale wace Asafu wokhala ku dzanja lace lamanja, ndiye Asafu mwana wa Berekiya, mwana wa Simeya,

40 mwana wa Mikaeli, mwana wa Baaseya, mwana wa Malikiya,

41 mwana wa Etini, mwana wa Zera, mwana wa Adaya,

42 mwana wal Edani, mwana wa Zima, mwana wa Simeyi,

43 mwana wa Yabati, mwana wa Gerisomu, mwana wa Levi.

44 Ndi ku dzanja lamanzere abale ao ana a Merari: Etani mwana wa Kisi, mwana wa Abidi, mwana wa Maluki,

45 mwana wa Hasabiya, mwana wa Amaziya, mwana wa Hilikiya,

46 mwana wa Amzi, mwana wa Bani, mwana wa Semeri,

47 mwana wa Mali, mwana wa Musi, mwana wa Merari, mwana wa Levi.

48 Ndi abale ao Alevi anaikidwa acite za utumiki ziti zonse za kacisi wa nyumba ya Mulungu.

49 Koma Aroni ndi ana ace adafofukiza pa guwa la nsembe yopsereza, ndi pa guwa la nsembe yofukiza, cifukwa ca nchito yonse ya malo opatulikitsa, ndi kucitira Israyeli cowatetezera, monga mwa zonse Mose mtumiki wa Mulungu adawauza.

50 Ndipo ana a Aroni ndiwo Eleazara mwana wace, Pinehasi mwana wace, Abisua mwana wace,

51 Buki mwana wace, Uzi mwana wace, Zerobiya mwana wace,

52 Merayoti mwana wace, Amariya mwana wace, Ahitubu mwana wace,

53 Zadoki mwana wace, Ahimaazi mwana wace.

54 Pokhala pao tsono monga mwa madera ao m'malire mwao ndi awa: kwa ana a Aroni a mabanja a Akobati, pakuti maere oyamba adagwera iwowa,

55 kwa iwo anapereka Hebroni m'dziko la Yuda, ndi podyetsa pace pozungulira pace;

56 koma minda ya mudzi ndi miraga yace anapatsa Kalebi mwana wa Yefune.

57 Ndi kwa ana a Aroni anapereka midzi yopulumukirako: Hebroni, ndi Libina ndi mabusa ace, ndi Yatiri, ndi Esitemowa ndi mabusa ace,

58 ndi Hileni ndi mabusa ace, ndi Debiri ndi mabusa ace,

59 ndi Asani ndi mabusa ace, ndi Betesemesi ndi mabusa ace;

60 ndi ku pfuko la Benjamini Geba ndi mabusa ace, ndi Alemeti ndi mabusa ace, ndi Anatoti ndi mabusa ace. Midzi yao yonse mwa mabanja ao ndiyo midzi khumi ndi itatu.

61 Ndipo otsala a ana a Kohati analandira mwa maere, motapa pa mabanja a pfuko, pa pfuko la Manase logawika pakati, midzi khumi.

62 Ndi kwa ana a Gerisomu monga mwa mabanja ao, motapa pa pfuko la Isakara, ndi pa pfuko la Aseri, ndi pa pfuko la Nafitali, ndi pa pfuko la Manase m'Basana, midzi khumi ndi itatu.

63 Ana a Merari analandira mwa maere monga mwa mabanja ao, motapa pa pfuko la Rubeni, ndi pa pfuko la Gadi, ndi pa pfuko la Zebuluni, midzi khumi ndi iwiri.

64 Ndipo ana a Israyeli anapatsa Alevi midzi ndi mabusa ao.

65 Ndipo anapatsa mwamaere, motapa pa pfuko la ana a Yuda, ndi pa pfuko la Simeoni, ndi pa pfuko la ana a Benjamini, midzi iyi yochulidwa maina ao.

66 Ndi mabanja ena a ana a Kohati anali nayo midzi ya malire ao, yotapa pa pfuko la Efraimu.

67 Ndipo anawapatsa midzi yopulumukiramo: Sekemu ndi mabusa ace ku mapiri a Efraimu, Gezeri ndi mabusa ace,

68 ndi Yokimeamu ndi mabusa ace, ndi Betihoroni ndi mabusa ace,

69 ndi Ayaloni ndi mabusa ace, ndi Gatirimoni ndi mabusa ace,

70 ndi motapa pa pfuko la Manase logawika pakati, Aneri ndi mabusa ace, ndi Bileamu ndi mabusa ace, kwa otsala a mabanja a ana a Kohati.

71 Ana a Gerisomu analandira motapa pa mabanja a pfuko la Manase logawika pakati, Golani m'Basana ndi mabusa ace, ndi Asitaroti ndi mabusa ace;

72 ndi motapa pa pfuko la Isakara, Kedesi ndi mabusa ace, Daberati ndi mabusa ace,

73 ndi Ramoti ndi mabusa ace, ndi Anemu ndi mabusa ace;

74 ndi motapa pa pfuko la Aseri, Masala ndi mabusa ace, ndi Abidoni ndi mabusa ace,

75 ndi Hukoki ndi mabusa ace, ndi Rehobu ndi mabusa ace;

76 ndi motapa pa pfuko la Nafitali, Kadesi m'Galileya ndi mabusa ace, ndi Hamoni ndi mabusa ace, ndi Kiriyataimu ndi mabusa ace.

77 Otsala a Alevi analandira, motapa pa pfuko la Zebuluni, Rimono ndi mabusa ace, Tabora ndi mabusa ace;

78 ndi tsidya lija la Yordano kum'mawa kwa Yordano analandira, motapa pa pfuko la Rubeni, Bezeri m'cipululu ndi mabusa ace, ndi Yaza ndi mabusa ace,

79 ndi Kedemoti ndi mabusa ace, ndi Mefati ndi mabusa ace;

80 ndi motapa m'pfuko la Gadi, Ramoti m'Gileadi ndi mabusa ace, ndi Mahanaimu ndi mabusa ace,

81 ndi Hezboni ndi mabusa ace, ndi Yazeri ndi mabusa ace.

7

1 Ana a Isakara ndiwo Tola, ndi Pua, Yasubu ndi Simironi; anai.

2 Ndi ana a Tola: Uzi, ndi Repaya, ndi Yerieli, ndi Yamai, ndi Ibsamu, ndi Semueli, akuru a nyumba za makolo; ao ndiwo a Tola, ngwazi zamphamvu, m'mibadwo yao; kuwerenga kwao masiku a Davide ndiko zikwi makumi awiri mphambu ziwiri kudza mazana asanu ndi limodzi.

3 Ndi mwana wa Uzi: Izrahiya; ndi ana a Izrahiya: Mikaeli, ndi Obadiya, ndi Yoeli, ndi Isiya; onse asanuwa ndiwo akuru.

4 Ndi pamodzi nao mwa mibadwo yao, mwa nyumba za makolo ao, panali magulu a nkhondo zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi cimodzi, popeza anacuruka akazi ao ndi ana ao.

5 Ndi abale ao mwa mabanja onse a Isakara, ngwazi zamphamvu, oyesedwa mwa cibadwidwe cao, onsewa ndiwo zikwi zisanu ndi zitatu mphambu zisanu ndi ziwiri.

6 Ana a Benjamini ndiwo Bela, ndi Bekeri, ndi Yedyaeli, atatu.

7 Ndi ana a Bela: Ezboni, ndi Uzi, ndi Uzieli, ndi Yerimoti, ndi hi, asanu; akuru a nyumba za makolo ao, ngwazi zamphamvu, owerengedwa m'mabuku a cibadwidwe zikwi makumi awiri mphambu ziwiri kudza makumi atatu ndi anai.

8 Ndi ana a Bekeri: Zemira, ndi Yoasi, ndi Eliezeri, ndi Eliunai, ndi Omri, ndi Yeremoti, ndi Abiya, ndi Anatoti, ndi Alemeti. Onsewa ndiwo ana a Bekeri.

9 Ndipo anayesedwa mwa cibadwidwe cao, mwa mibadwo yao, akulu a nyumba za makolo ao, ngwazi zamphamvu zikwi makumi awiri mphambu mazana awiri.

10 Ndi mwana wa Yedyaeli: Bilani; ndi ana a Bilani: Yeusi, ndi Benjamini, ndi Ehudi, ndi Kenana, ndi Zetani, ndi Tarasisi, ndi Ahisabara.

11 Onsewa ndiwo ana a Yedyaeli; ndiwo akuru a nyumba za makolo ao, ngwazi zamphamvu zikwi khumi mphambu zisanu ndi ziwiri kudza mazana awiri akuturuka kugulu kunkhondo.

12 Sufimu yemwe ndi Hupimu ana a Iri, ndi Husimu mwana wa Aheri.

13 Ana a Nafuali: Yazieli, ndi Guni, ndi Yezeri, ndi Salumu, ana a Bila.

14 Ana a Manase ndiwo Asrieli amene mkazi wace anambala, Koma mkazi wace wamng'ono Maramu anabala Makiri atate wa Gileadi;

15 ndi Makiri anadzitengera mkazi, mlongo wace wa Hupimu ndi Supimu, dzina lace ndiye Maaka. Ndipo dzina la mwana waciwiri wa Manase ndiye Tselofekadi. Ndi Tselofekadi anali ndi ana akazi.

16 Ndi Maaka mkazi wa Makiri anabala mwana, namucha dzina lace Peresi, ndi dzina la mbale wace ndiye Seresi, ndi ana ace ndiwo Ulamu, ndi Rakemu.

17 Ndi mwana wa Ulamu: Bedani; ndiwo ana a Gileadi mwana wa Makiri mwana wa Manase.

18 Ndi mlongo wace Hamoleketi anabala Isodi, ndi Abiezeri, ndi Mala.

19 Ndi ana a Semida ndiwo Ahiani, ndi Sekemu, ndi Liki, ndi Aniamu.

20 Ndi ana a Efraimu: Sutera, ndi Beredi mwana wace, ndi Tahati mwana wace, ndi Ekada mwana wace, ndi Tahati mwana wace,

21 ndi Zabadi mwana wace, ndi Sutela mwana wace, ndi Ezeri, ndi Eleadi, amene anthu a Gadi obadwa m'dziko anamupha, popeza anatsikira kukalanda zoweta zao.

22 Ndipo Efraimu atate wao, anacita maliro masiku ambiri, ndi abale ace anadza kudzamtonthoza mtima.

23 Ndipo analowa kwa mkazi wace, naima iye, nabala mwana, namucha dzina lace Beriya, popeza m'nyumba mwace mudaipa.

24 Ndipo mwana wace wamkazi ndiye Seera, amene anamanga Beti-horoni wa kunsi, ndi Beti-horoni wa kumtunda, ndi Uzeniseera.

25 Ndipo Refa anali mwana wace, ndi Resefe, ndi Tela mwana wace, ndi Tahani mwana wace,

26 Ladana mwana wace, Amihudi mwana wace, Elisamu mwana wace,

27 Nuni mwana wace, Yoswa mwana wace.

28 Ndipo dziko lao, ndi pokhala pao ndizo Beteli ndi miraga yace, ndi kum'mawa Narani, ndi kumadzulo Gezeri ndi miraga yace, ndi Sekemu ndi miraga yace, mpaka Aza ndi miraga yace;

29 ndi kumalire a ana a Manase; Beteseani ndi miraga yace, Taanaki ndi miraga yace, Megido ndi miraga yace, Dora ndi miraga yace. M'menemo anakhala ana a Yosefe mwana wa Israyeli.

30 Ana a Aseri: Imna, ndi Isva, ndi Isvi, ndi Beriya, ndi Sera mlongo wao.

31 Ndi ana a Beriya: Heberi, ndi Malikieli, ndiye atate wa Birizaiti.

32 Ndi Heberi anabala Yafteti, ndi Someri, ndi Hotamu, ndi Suwa mlongo wao.

33 Ndi ana a Yafteti: Pasaki, ndi Bimali, ndi Asvati. Awa ndi ana a Yafteti.

34 Ndi ana a Semeri: Ahi, ndi Roga, Yehuba, ndi Aramu.

35 Ndi ana a Helemu mbale wace: Zofa, ndi Imna, ndi Selesi, ndi Amali.

36 Ana a Zofa: Suwa, ndi Harineferi, ndi Sauli, ndi Beri, ndi Imra,

37 Bezeri, ndi Hndi, ndi Sama, ndi Silisa, ndi Itirani, ndi Beera.

38 Ndi ana a Yeteri: Yefune, ndi Pisipa, ndi Ara.

39 Ndi ana a Ula: Ara, ndi Hanieli, ndi Rizya.

40 Awa onse ndiwo ana a Aseri, akuru a nyumba za makolo ao, ngwazi zosankhika ndi zamphamvu, akuru mwa akalonga. Oyesedwa mwa cibadwidwe cao otumikira kunkhondo ndiwo amuna zikwi makumi awiri mphambu zisanu ndi cimodzi.

8

1 Ndipo Benjamini anabala Bela mwana wace vyoyamba, Asibeli waciwiri, ndi Ahara wacitatu,

2 Noha wacinai, ndi Rafa wacisanu.

3 Ndi Bela anali ndi ana: Adara, ndi Gera, ndi Abihudi,

4 ndi Abisuwa, ndi Namani, ndi Ahowa,

5 ndi Gera, ndi Sefufani, ndi Huramu.

6 Ndi ana a Ehudi ndi awa: ndiwo akuru a nyumba za makolo ao a iwo okhala ku Geba, ndipo anawatenga ndende kumka ku Manahati,

7 natenga ndende Namani, ndi Ahiya, ndi Gera, ndipo, anabala Uza, ndi Ahihudi.

8 Ndipo Saharaimu anabala ana ku dziko la Moabu, atacotsa akazi ace Husimu ndi Baara.

9 Ndipo Hodesi mkazi wace anambalira Yohabu, ndi Zibiya, ndi Mesa, ndi Malikamu,

10 ndi Yeuzi, ndi Sakiya, ndi Mirima. Awa ndi ana ace akurua nyumbazamakolo ao.

11 Ndi Husimu anambalira Abitubu, ndi Elipaala.

12 Ndi ana a Elipaala: Eberi, ndi Misamu, ndi Semedi, amene anamanga Ono, ndi Ludi ndi miraga yace,

13 ndi Beriya, ndi Sema; ndiwo akuru a nyumba za makolo a iwo okhala m'Ayaloni, amene anathawitsa okhala m'Gati;

14 ndi Ahio, Sasaki, ndi Yeremoti,

15 ndi Zebadiya, ndi Aradi, ndi Ederi,

16 ndi Mikaeli, ndi Isipa, ndi Yoha, ana a Beriya;

17 ndi Zebadiya, ndi Mesulamu, ndi Hiziki, ndi Heberi,

18 ndi Ismerai, ndi Izliya, ndi Yobabu, ana a Elipaala;

19 ndi Yakimu, ndi Zikiri, ndi Zabidi,

20 ndi Elianai, ndi Ziletai, ndi Elieli,

21 ndi Adaya, ndi Beraya, ndi Simirati, ana a Simei;

22 ndi Isipani, ndi Eberi, ndi Elieli,

23 ndi Abidoni, ndi Zikiri, ndi Hanani,

24 ndi Hananiya, ndi Elamu, ndi Antotiya,

25 ndi Ifideya, ndi Penueli, ana a Sasaki;

26 ndi Samserai, ndi Sehariya, ndi Ataliya,

27 ndi Yaaresiya ndi Eliya, ndi Zikiri, ana a Yerohamu.

28 Awa ndi akuru a nyumba za makolo mwa mibadwo yao, ndiwo akuru anakhala m'Yerusalemu awa.

29 Ndipo m'Gibeoni anakhala atate a Gibeoni, dzina la mkazi wace ndiye Maaka;

30 ndi mwana wace woyamba ndiye Abidoni, opondana naye ndi Zuri, ndi Kisi, ndi Baala, ndi Nadabu,

31 ndi Gedoro, ndi Ahiyo, ndi Zekeri.

32 Ndipo Mikiloti anabala Simeya. Ndi iwonso anakhala pamodzi ndi abale ao m'Yerusalemu, popenyana ndi abale ao.

33 Ndipo Neri anabala Kisi, ndi Kisi anabala Sauli, ndi Sauli anabala Yonatani, ndi Malikisuwa, ndi Abinadabu, ndi Esibaala.

34 Ndi mwana wa Yonatani ndiye Meri-baala; ndi Meri-baala anabala Mika.

35 Ndi ana a Mika: Pitoni, ndi Meleki, ndi Tareya, ndi Ahazi.

36 Ndi Ahazi anabala Yehoada, ndi Yehoada anabala Alemeti, ndi Azimaveti, ndi Zimri; ndi Zimri anabala Moza;

37 ndi Moza anabala Bineya, mwana wace ndiye Rafa, mwana wace Eleasa, mwana wace Azeli;

38 ndipo Azeli anali nao ana asanu ndi mmodzi, maina ao ndiwo Azrikamu, Bokeru, ndi Ismayeli, ndi Seariya, ndi Obadiya, ndi Hanani. Onsewa ndiwo ana a Azeli.

39 Ndi ana a Ezeki mbale wace: Ulamu mwana wace woyamba, Yeusi waciwiri, ndi Elifeleti wacitatu.

40 Ndipo ana a Ulamu ndiwo ngwazi zamphamvu, ndiwo oponya mibvi, nakhala nao ana ambiri ndi zidzukulu zana limodzi. Onsewa ndiwo a ana a Benjamini.

9

1 Ndipo Aisrayeli onse anawerengedwa mwa cibadwidwe cao; ndipo taonani, alembedwa m'buku la mafumu a Israyeli; ndipo Yuda anatengedwa ndende kumka ku Babulo cifukwa ca kulakwa kwao.

2 Okhala m'dziko oyamba tsono, akukhala mwao mwao m'roidzi mwao, ndiwo Israyeli, ansembe, Alevi, ndi Anetini.

3 Ndipo m'Yerusalemu munakhala a ana a Yuda, ndi a ana a Benjamini, ndi a ana a Efraimu ndi Manase:

4 Utai mwana wa Amihudi, mwana wa Omri, mwana wa Imri, mwana wa Bani, wa ana a Perezi mwana wa Yuda.

5 Ndipo a Asiloni: Asaya woyamba, ndi ana ace.

6 Ndi a ana a Zera: Yeueli ndi abale ao mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi anai.

7 Ndi a ana a Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Hodavia, mwana wa Hasenuwa;

8 ndi Ibineya mwana wa Yerohamu, ndi Ela mwana wa Uzi, mwana-wa Mikiri, ndi Mesulamu mwana wa Sefatiya, mwana wa Reueli, mwana wa Ibniya,

9 ndi abale ao monga mwa mibadwo yao mazana asanu ndi anai mphambu makumi asanu kudza asanu ndi mmodzi. Onsewa ndiwo akuru a nyumba za makolo ao m'nyumba za makolo ao.

10 Ndi a ansembe: Yedaya, ndi Yehoyaribu, ndi Yakini,

11 ndi Azariya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubu, mtsogoleri wa m'nyumba ya Mulungu;

12 ndi Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pasuri, mwana wa Malikiya, ndi Maasai mwana wa Adieli, mwana wa Yazera, mwana wa Mesulamu, mwana wa Mesilemiti, mwana wa Imeri,

13 ndi abale ao, akuru a nyumba za makolo ao cikwi cimodzi mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu ndi limodzi, anthu odziwitsitsa Debito ya utumiki wa nyumba ya Mulungu.

14 Ndi a Alevi: Semaya mwana wal Hasubu, mwana wa Azrikamu, mwana wa Hasabiya, a ana a Merari;

15 ndi Bakabakara, Heresi, ndi Galala, ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zikiri, mwana wa Asafu;

16 ndi Obadiya mwana wa Semaya, mwana wa Galala, mwana wa Yedutuni, ndi Berekiya mwana wa Asa, mwana wa Elikana, wokhala m'midzi ya Anetofati.

17 Ndi odikira pakhomo: Salumu, ndi Akubu, ndi Talimoni, ndi Ahimani ndi abate ao; Salumu ndi mkuru wao,

18 amene adadikira pa cipata ca mfumu kum'mawa mpaka pomwepo, ndiwo odikira pakhomo a tsasa la ana a Levi.

19 Ndipo Salumu mwana wa Kore, mwana wa Ebiasafu; mwana wa Kora, ndi abale ace a nyumba ya atate wace; Akora anayang'anira nchito ya utumiki, osunga zipata za kacisi monga makolo ao; anakhala m'cigono ca Yehova osunga polowera;

20 ndi a Pinehasi mwana wa Eleazara anali mtsogoleri wao kale, ndipo Yehova anali naye.

21 Zekariya mwana wa Meselemiya anali wodikira pakhomo pa cihema cokomanako.

22 Iwo onse osankhidwa akhale odikira kuzipata ndiwo mazana awiri mphambu khumi ndi awiri. Iwo anawerengedwa monga mwa cibadwidwe cao, m'midzi mwao, amene Davide ndi Samueli mlauli anawaika m'udindo wao.

23 Momwemo iwo ndi ana ao anayang'anira zipata za ku nyumba ya Yehova, ndiyo nyumba ya kacisi, m'udikiro wao.

24 Pa mbali zinai panali odikira kum'mawa, kumadzulo, kumpoto, ndi kumwela.

25 Ndi abale ao m'midzi mwao akafikafika, atapita masiku asanu ndi awiri masabata onse, kuti akhale nao;

26 pakuti odikira anai akuru, ndiwo Alevi, anali m'udindo wao, nayang'anira zipinda ndi mosungiramo cuma m'nyumba ya Mulungu.

27 Ndipo amagona usiku m'zipinda zozinga nyumba ya Mulungu, popeza udikiro wace ndi wao; kuitsegula m'mawa ndi m'mawa ndi kwaonso.

28 Ndi ena a iwo anayang'anira zipangizo za utumikiwo, pakuti analowa nazo ataziwerenga, naturuka nazo ataziwerenga.

29 Ndi ena a iwo anaikidwa ayang'anire zipangizo ziti zonse, ndi zipangizo zonse za malo opatulika, ndi ufa wosalala, ndi vinyo, ndi mafuta, ndi libano, ndi zonunkhira.

30 Ndi ana ena a, ansembe anasanganiza cisanganizo ca zonunkhira,

31 Ndi Matitiya wina wa Alevi, ndiye mwana woyamba wa Salumu Mkora, anaikidwa ayang'anire zokazingidwa m'ziwaya.

32 Ndi ena a abale ao, a ana a Akohati, anayang'anira mkate woonekera, kuukonza masabata onse.

33 Ndipo awa ndi oyimba akuru a nyumba za makolo a Alevi, okhala m'zipinda, omasuka ku nchito zina; pakuti anali nayo nchito yao usana ndi usiku.

34 Awa ndi akuru a nyumba za makolo a Alevi mwa mibadwo yao, ndiwo akuru; anakhala ku Yerusalemu awa.

35 Ndipo m'Gibeoni munakhala atate wa Gibeoni Yeieli, dzina la mkazi wace ndiye Maaka;

36 ndi mwana wace woyamba ndiye Abidoni, opandana naye ndi Zuri, ndi Kisi, ndi Baala, ndi Neri, ndi Nadabu,

37 ndi Gedoro, ndi Ahiya, ndi Zekariya, ndi Mikiloti.

38 Ndi Mikiloti anabala Simeamu. Ndipo iwonso anakhala pamodzi ndi abale ao m'Yerusalemu, pandunji pa abale ao.

39 Ndipo Neri anabala Kisi, ndi Kisi anabala Sauli, ndi Sauli anabala Yonatani, ndi Malikisuwa, ndi Abinadabu, ndi Esbaala.

40 Ndipo mwana wa Yonatani ndiye Meribaala; ndi Meribaala anabala Mika.

41 Ndi ana a Mika: Pitoni, ndi Meleki, ndi Tareya, ndi Ahazi.

42 Ndi Ahazi anabala Yara, ndi Yara anabala Ameleti, ndi Azmaveti, ndi Zimri; ndi Zimri anabala Moza,

43 ndi Moza anabala Bineya, ndi Refaya mwana wace, Eleasa mwana wace; Azeli mwana wace;

44 ndi Azeli anali nao ana asanu ndi mmodzi, maina ao ndi awa; Azrikamu, Bokeru, ndi Ismayeli, ndi Seariya, ndi Obadiya, ndi Hanani; awa ndi ana a Azeli.

10

1 Afilisti tsono analimbana nkhondo ndi Israyeli; ndipo amuna a Israyeli anathawa pamaso pa Afilisti, nagwa ophedwa pa phiri la Giliboa.

2 Ndipo Afilisti anaumirira kutsata Sauli ndi ana ace, ndi Afilistiwo anawapha Yonatani, ndi Abinadabu, ndi Malikisuwa, ana a Sauli.

3 Ndi nkhondoyi inamkulira Sauli, ndi amauta anampeza; ndipo anatenga nkhawa cifukwa ca amauta.

4 Pamenepo Sauli anati kwa wonyamula zida zace, Solola lupanga lako, nundipyoze nalo, angafike osadulidwa awa ndi kundiseka, Koma wonyamula zida zace anakana, popeza anaopa kwambiri. Pomwepo Sauli anatenga lupanga lace, naligwera.

5 Ndipo pamene wonyamula zida zace anaona kuti Sauli wafa, anagwera nayenso lupanga lace, nafa.

6 Momwemo anafa Sauli, ndi ana ace atatu; ndi nyumba yace yonse idafa pamodzi.

7 Ndipo pamene amuna onse a Israyeli okhala m'cigwamo anaona kuti anathawa, ndi kuti Sauli ndi ana ace adafa, anasiya midzi yao, nathawa; nadza Afilisti, nakhala m'menemo.

8 Ndipo m'mawa mwace anafika Afilisti kubvula za ophedwa, napeza Sauli ndi ana ace adagwa pa phiri la Giliboa.

9 Ndipo anambvula natenga mutu wace, ndi zida zace, natumiza ku dziko la Afilisti pozungulirapo, kulalika m'mafano ao ndi mwa anthu.

10 Ndipo anaika zida zace m'nyumba ya milungu yao, napacika mutu wace m'nyumba ya Dagoni.

11 Ndipo onse a Yabesi Gileadi, atamva zonse Afilisti adacitira Sauli,

12 anauka ngwazi zonse, nacotsa mtembo wa Sauli, ndi mitembo ya ana ace, nabwera nayo ku Yabesi, naika mafupa ao patsinde pa mtengo wathundu ku Yabesi, nasala masiku asanu ndi awiri.

13 Momwemo Sauli anafa, cifukwa ca kulakwa kwace analakwira Yehova, kulakwira mau a Yehova amene sanawasunga; ndiponso cifukwa ca kufunsira wobwebweta, kufunsirako,

14 osafunsira kwa Yehova; cifukwa cace anamupha, napambutsira ufumu kwa Davide mwana wa Jese.

11

1 Pamenepo Aisrayeli onse anasonkhana kwa Davide ku Hebroni, ndi kuti, Taonani, ife ndife pfupa lanu, ndi mnofu wanu.

2 Ngakhale kale lomwe, pokhala mfumu Sauliyo, woturuka ndi kulowa nao Aisrayeli ndinu; ndipo Yehova Mulungu wanu anati kwa inu, Uzidyetsa anthu anga Aisrayeli, nukhale mtsogoleri wa anthu anga Israyeli.

3 Akuru onse omwe a Israyeli anadza kwa mfumu ku Hebroni; ndipo Davide anapangana nao pangano ku Hebroni pamaso pa Yehova; ndipo anamdzoza Davide akhale mfumu ya Israyeli monga mwa mau a Yehova, ndi lizanja la Samueli.

4 Namuka Davide ndi Aisrayeli onse naye ku Yerusalemu, ndiwo Yebusi; ndipo Ayebusi nzika za m'dziko zinali komweko.

5 Ndipo nzika za m'Yebusi zinati kwa Davide, Sungalowe muno. Koma Davide analanda linga la Ziyoni, ndiwo mudzi wa Davide.

6 Nati Davide, Ali yense woyamba kukantha Ayebusi, yemweyo adzakhala mkulu ndi mtsogoleri. Nayamba kukwerako Yoabu mwana wa Zeruya, nakhala mkuru iyeyu.

7 Ndipo Davide anakhala m'lingamo; cifukwa cace analicha mudzi wa Davide.

8 Ndipo anamanga mudzi pozungulira pace, kuyambira ku Milo ndi pozungulira pace; ndi Yoabu anakonzanso potsala pa mudzi.

9 Ndipo Davide anakula-kulabe, pakuti Yehova wa makamu anali naye.

10 Akuru a amphamvu aja Davide anali nao akulimbika pamodzi naye m'ufumu wace, pamodzi ndi Aisrayeli onse, kumlonga ufumu, monga mwa mau a Yehova akunena za Israyeli, ndi awa.

11 Kuwerenga kwa amphamvu aja Davide anali nao ndi uku: Yasobeamu mwana wa Mhakimoni, mkuru wa makumi atatu aja, anasamulira mazana atatu mkondo wace, nawapha nthawi imodzi.

12 Ndi pambuyo pace Eleazara mwana wa Dodo M-ahohi, ndiye mmodzi wa atatu aja amphamvu.

13 Anali pamodzi ndi Da vide ku Pasidamimu muja; Afilisti anasonkhanako kunkhondo kumene kunali munda wodzala ndi barele; ndipo anthu anathawa pamaso pa Afilisti.

14 Koma anadziimika pakati pa munda, naulanditsa, nakantha Afilisti; m'mwemo anawapulumutsa Yehova ndi cipulumutso cacikuru.

15 Ndipo atatu a akuru makumi atatu anatsikira kuthanthwe kwa Davide, ku phanga la Adulamu; ndi nkhondo ya Afilisti idamanga misasa m'cigwa ca Refaimu.

16 Pamenepo Davide anali m'linga, ndi boma la askari linali ku Betelehemu.

17 Ndipo Davide analakalaka, nati, Ha! mwenzi wina atandimwetsa madzi a m'citsime ca ku Betelehemu ciri kucipata,

18 Napyola atatuwo misasa ya Afilish natunga madzi ku citsime ca ku Betelehemu ciri kucipata, nabwera nao kwa Davide; koma Davide anakana kumwako, koma anawathirira kwa Yehova;

19 nati, Pali Mulungu wanga, kukhale kutali kwa ine kucita ici. Ngati ndidzamwa mwazi wa anthu awa? Akadataya moyo wao, inde akadataya moyo wao, pakukatenga madziwa. M'mwemo sanafuna kuwamwa. Izi anazicita atatu amphamvuwa.

20 Ndipo Abisai mbale wa Yoabu, ndiye wamkuru wa atatuwa; pakuti anasamulira mazana atatu mkondo wace, nawapha, namveka dzina pakati pa atatuwa.

21 Mwa atatuwa iye anali waulemu woposa awiriwa, nasanduka mkuru wao; koma sanafikana nao atatu oyamba aja.

22 Benaya mwana wa Yehoyada, mwana wa ngwazi ya ku Kabzeeli, wocita zazikuru, anapha ana awiri a Ariyeli wa ku Moabu; anatsikanso, napha mkango m'kati mwa dzenje nyengo ya cipale cofewa.

23 Anaphanso M-aigupto munthu wamkuru, msinkhu wace mikono isanu, ndi m'dzanja la M-aigupto munali mkondo ngati mtanda woombera nsaru; ndipo anamtsikira ndi ndodo, nakwatula mkondo m'dzanja la M-aigupto, namupha ndi mkondo wace womwe.

24 Izi anazicita Benaya mwana wa Yehoyada, namveka dzina mwa atatu amphamvuwo.

25 Taonani, anali wa ulemu woposa makumi atatuwo, koma sanafikana atatu oyamba aja; ndipo Davide anamuika mkuru wa olindirira ace.

26 Ndipo amphamvuwo a magulu a nkhondo ndiwo Asaheli mbale wa Yoabu, Elanani mwana wa Dodo wa ku Betelehemu,

27 Samoti Mharori, Helezi Mpeloni,

28 Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekoi, Abiezeri wa ku Anatoti,

29 Sibekai Mhusati, liai M-ahohi,

30 Maharai Mnetofati, Heledi mwana wa Bana Mnetofati,

31 Itai mwana wa Ribai wa Gibeya wa ana a Benjamini, Benaya Mpiratoni,

32 Horai wa ku mitsinje ya Gaasi, Abiyeli M-ariba,

33 Azmaveti Mbaharumi, Eliaba Mshaliboni;

34 ana a Hasemu Mgizoni; Yonatani mwana wa Sage Mharari,

35 Ahiamu mwana wa Sakari Mharari, Elifali mwana wa Uri,

36 Heferi Mmekerati, Ahiya Mpeloni,

37 Hezro wa ku Karimeli, Naarai mwana wa Ezbai,

38 Yoeli mbale wa Natani, Mibari mwana wa Hagiri,

39 Zeleki M-amoni, Naharai Mberoti wonyamula zida za Yoabu mwana wa Zeruya,

40 Ira M-itiri, Garebi M-itiri,

41 Uriya Mhiti, Zabadi mwana wa Alai,

42 Adina mwana wa Siza Mrubeni mkuru wa Arubeni, ndi makumi atatu pamodzi naye,

43 Hanani mwana wa Maaka, ndi Yosafati Mmitini,

44 Uziya M-asterati, Sama ndi Yeieli ana a Hotamu wa ku Aroeri,

45 Yedyaeli mwana wa Simri, ndi Yoha mbale wace Mtizi,

46 Elieli Mmahavi, ndi Yeribai ndi Yosaviya ana a Elinaamu, ndi Itima Mmoabu,

47 Elieli, ndi Obedi, ndi Yasiyeli Mmezobai.

12

1 Anadzawo kwa Davide ku Zikilaga, akali citsekedwere cifukwa ca Sauli mwana wa Kisi, ndi awa; ndiwo mwa amphamvuwo omthandiza kunkhondo.

2 Anakoka mauta; naponya miyala, naponya mibvi ndi uta ndi dzanja lamanja ndi lamanzere lomwe; ndiwo a abale ace a Sauli, Abenjamini.

3 Mkuru wao ndiye Ahiezeri, ndi Yoasi, ana a Semaa wa ku Gibeya; ndi Yezieli, ndi Peleti, ana a Azmaveti; ndi Beraka, ndi Yehu wa ku Anatoti,

4 ndi Ismaya wa ku Gibeoni, wamphamvu mwa makumi atatuwo ndi woyang'anira makumi atatuwo, ndi Yeremiya, ndi Yahazieli, ndi Yohanani, ndi Yozabadi wa ku Gedera,

5 Eluzai, ndi Yerimoti, ndi Bealiya, ndi Semariya, ndi Sefatiya wa ku Harupi,

6 Elikana, ndi Isiya, ndi Azereli, ndi Yoezeri, ndi Yasobeamu ndiwo Akora;

7 ndi Yoda, ndi Zebadiya, ana a Yerohamu wa ku Gedoro.

8 Ndi Agadi ena anapambukira kwa Davide ku liogala m'cipululu, ngwazi zamphamvu zozerewera nkhondo, zogwira cikopa ndi mkondo; nkhope zao zikunga nkhope za mikango, ndi liwiro lao longa la ngoma kumapiri:

9 Ezeri mkuru wao, waciwiri Obadiya, wacitatu Eliabu,

10 wacinai Misimana, wacisanu Yeremiya,

11 wacisanu ndi cimodzi Atai, wacisanu ndi ciwiri Elieli,

12 wacisanu ndi citatu Yohanani, wacisanu ndi cinai Elzabadi,

13 wakhumi Yeremiya, wakhumi ndi cimodzi Makibanai.

14 Awa a ana a Gadi, anali atsogoleri a nkhondo; wamng'ono wa iwo anayang'anira zana limodzi, ndi wamkuru wa iwo anayang'anira cikwi cimodzi.

15 Awa ndi omwe aja anaoloka Yordano mwezi woyamba, atadzala kusefukira magombe ace onse; nathawitsa onse okhala m'zigwa kum'mawa ndi kumadzulo.

16 Ndipo anadza ena a ana a Benjamini ndi Yuda kulinga kwa Davide.

17 Ndipo Davide anaturuka kukomana nao, nayankha, nanena nao, Ngati mwandidzera mwamtendere kundithandiza, mtima wanga udzalumikizana nanu; koma ngati mwafika kundipereka kwa adani anga, popeza m'manja mwanga mulibe ciwawa, Mulungu wa makolo athu acione ndi kucilanga.

18 Pamenepo mzimu unabvala Amasai, ndiye wamkuru wa makumi atatuwo, nati iye, Ndife anu, Davide, tibvomerezana nanu mwana wa Jese inu: mtendere, mtendere ukhale ndi inu, ndi mtendere ukhale ndi athandizi anu; pakuti Mulungu wanu akuthandizani. Ndipo Davide anawalandira, nawaika akuru a magulu.

19 Ena a Manase omwe anapambukira kwa Davide, muja iye anadza ndi Afilisti koponyana nkhondo ndi Sauli, koma sanawathandiza; popeza akalonga a Afilisti, atacita upo, anamuuza acoke, ndi kuti, Adzapambukira kwa mbuye wace Sauli ndi kutisandulikira.

20 Pomuka iye ku Zikilaga anapambukira kwa iye a Manase: Adina, ndi Yozabadi, ndi Yedyaeli, ndi Mikaeli, ndi Yozabadi, ndi Elihu, ndi Ziletai, akuru a zikwi a ku Manase.

21 Ndipo anathandiza Davide aponyane nalo gulu la acifwamba, pakuti onse ndiwo ngwazi zamphamvu, nakhala atsogoleri m'khamu la nkhondo.

22 Pakuti nthawi yomweyo anadza kwa Davide kumthandiza, mpaka kunali nkhondo yaikuru; ngati nkhondo ya Mulungu.

23 Ndipo kuwerenga kwa akuru okonzekeratu kunkhondo, anadzawo kwa Davide ku Hebroni, kupambukitsa ufumu wa Sauli ukhale wace, monga mwa mau a Yehova, ndi: uku.

24 Ana a Yuda akunyamula zikopa ndi mikondo ndiwo zikwi zisanu ndi cimodzi mphambu mazana asanu ndi atatu, okonzekeratu kunkhondo.

25 A ana a Simeoni ngwazi zamphamvu za nkhondo zikwi zisanu ndi ziwiri mphambu zana liimodzi.

26 A ana a Levi zikwi zinai mphambu mazana asanu ndi limodzi.

27 Ndipo Yehoyada, ndiye mtsogoleri wa Aaroni, ndi pamodzi nave zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi awiri;

28 ndi Zadoki, ndiye mnyamata, ngwazi yamphamvu, ndi a nyumba ya kholo lace, akuru makumi awiri mphambu awfri.

29 Ndi a ana a Benjamini, abale a Sauli, zikwi zitatu; pakuti mpaka pomwepo ocuruka a iwowa anaumirira nyumba ya Sauli.

30 Ndi a ana a Efraimu zikwi makumi awiri mphambu mazana asanu ndi atatu, ngwazi zamphamvu, anthu omveka m'nyumba za makolo ao.

31 Ndipo a pfuko la Manase logawika pakati zikwi khumi mphambu zisanu ndi zitatu, ochulidwa maina ao kuti adzalonge Davide mfumu.

32 Ndi a ana a Isakara, anthu akuzindikira nyengo, akudziwa zoyenera Israyeli kuzicita, akuru ao ndiwo mazana awiri; ndi abale ao onse anapenyerera pakamwa pao.

33 A Zebuloni akuturuka kukhamu, opangira nkhondo, monga mwa zida ziri zonse za nkhondo, zikwi makumi asanu, akusunga malongosoledwe a nkhondo ndi mtima wosatekeseka.

34 Ndi a Nafitali atsogoleri cikwi cimodzi, ndi pamodzi nao ogwira zikopa ndi mikondo zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi ziwiri.

35 Ndi a Adani akupangira nkhondo zikwi makumi awiri mphambu zisanu ndi zitatu kudza mazana asanu ndi limodzi.

36 Ndi a Aseri akuturuka kukhamu, akupangira nkhondo, zikwi makumi anai.

37 Ndi tsidya lga la Yordano a Arubeni, ndi Agadi, ndi pfuko la: Manase logawika pakati, ndi zida: ziri zonse za khamu kucita nazo nkhondo, zikwi zana limodzi ndi makumi awiri.

38 Onsewa, ndiwo anthu a nkhondo akusunga malongosoledwe a nkhondo, anadza ku Hebroni ndi mtima wangwiro kudzamlonga Davide mfumu ya Aisraeli onse; ndi onse otsala a Israyeli omwe anali a mtima umodzi kumlonga Davide ufumu.

39 Ndipo anali komweko kwa Davide masiku atatu kudya ndi kumwa, popeza abale ao-anazikonzeratu.

40 Ndiponso akuyandikizana nao mpaka Isakara ndi Zebuloni ndi Nafitali anabwera nao mkate osenzetsa aburu, ndi ngamira, ndi nyuru, ndi ng'ombe, zakudya zaufa, ndi ncinci zankhuyu, ndi ncinci zamphesa, ndi vinyo, ndi mafuta, ndi ng'ombe, ndi nkhosa zocuruka; pakuti munali cimwemwe m'Israyeli.

13

1 Ndipo Davide anafunsana ndi akuru a zikwi ndi a mazana, inde atsogoleri ali onse.

2 Ndipo Davide anati kwa msonkhano wonse wa Israyeli, Cikakomera inu, ndipo cikacokera kwa Yehova Mulungu wathu, titumize konse kuti abale athu otsala m'dziko lonse la Israyeli, ndi ansembe ndi Alevi okhala nao m'midzi yao yokhala napa podyetsa, kuti asonkhane kwa ife;

3 ndipo tibwere nalo kwa ife likasa la Mulungu wathu, pakuti sitinafunako masiku a Sauli.

4 Ndipo a msonkhano onse anati kuti adzacita; pakuti cidayenera cinthuci pamaso pa anthu onse.

5 M'mwemo Davide anamemeza Aisrayeli onse kuyambira Sihori wa ku Aigupto mpaka polowera ku Hamati, kutenga likasa la Mulungu ku Kiriati-Yearimu.

6 Ndipo Davide ndi Aisrayeli onse pamodzi naye anakwera kumka ku Baala, ndiko ku Kiriati-Yearimu wa m'Yuda, kukwera nalo kucokera komweko likasa la Mulungu Yehova wakukhala pa akerubi, kumene aitanirako Dzina.

7 Ndipo anatengera likasa la Mulungu pa gareta watsopano kucokera ku nyumba ya Abinadabu; ndi Uza ndi Ahiyo anayendetsa ng'ombe za pa garetayo,

8 Ndipo Davide ndi Aisrayeli onse anasewera pamaso pa Mulungu ndi mphamvu yao yonse; ndi nyimbo, ndi azeze, ndi zisakasa, ndi malingaka, ndi nsanje, ndi malipenga,

9 Ndipo pamene anafika ku dwale la Kidoni, Uza anatambasula dzanja lace kulicirikiza likasa, pakuti ng'ombe zikadapulumuka.

10 Ndi mkwiyo wa Yehova unayakira Uza, namkantha, cifukwa anatambasulira likasa dzanja lace, nafa komweko pamaso pa Mulungu.

11 Ndipo kudaipira Davide kuti Yehova adacita cipasulo ndi Uza; motero anacha malowo Perezi Uza, mpaka lero lino.

12 Ndipo Davide anaopa Mulungu tsikulo, ndi kuti, Ndidzafika nalo bwanji likasa la Mulungu kwathu?

13 M'mwemo Davide sanafika nalo likasa kwao ku mudzi wa Davide, koma analipambutsira ku nyumba ya Obedi Edomu wa ku Giti.

14 Ndi likasa la Mulungu linakhala ndi banja la Obedi Edomu m'nyumba mwace miyezi itatu; ndipo Yehova anadalitsa nyumba ya Obedi Edomu, ndi zonse anali nazo.

14

1 Ndipo Hiramu mfumu ya Turo anatumiza mithenga kwa Davide, ndi mikungudza, ndi amisiri omanga miyala, ndi amatabwa, kuti ammangire nyumba.

2 Ndipo Davide anazindikira kuti Yehova adamkhazikitsa mfumu ya Israyeli; pakuti ufumu wace unakwezekadi, cifukwa ca anthu ace Israyeli.

3 Ndipo Davide anatenga akazi ena ku Yerusalemu, nabala Davide ana amuna ndi akazi ena.

4 Maina a ana anali nao m'Yerusalemu ndi awa: Samna, ndi Sobabu Natani, ndi Solomo,

5 ndi Ibara, ndi Elisua, ndi Elipeleti,

6 ndi Noga, ndi Nefegi, ndi Yafiya,

7 ndi Elisama, ndi Beliyada, ndi Elifeleti.

8 Pamene Afilisti anamva kuti anamdzoza Davide akhale mfumu ya Aisrayeli onse, Afilisti onse anakwera kufunafuna Davide; ndipo Davide anamva, nawaturukira.

9 Afilisti tsono anafika, nafalikira m'cigwa ca Refaimu.

10 Ndipo Davide anafunsira kwa Mulungu, kun, Ndikwere kodi kuyambana ndi Afilisti? mudzawapereka m'dzanja langa kodi? Ndipo Yehova anati kwa iye, Kwera, pakuti ndidzawapereka m'dzanja lako.

11 Atafika tsono ku Baala Perazimu, Davide anawakantha komweko; nati Davide, Mulungu anapasula adani anga ndi dzanja langa, ngati pokhamulira madzi. Cifukwa cace analicha dzina la malowo Baala Perazimu.

12 Ndipo anasiyako milungu yao; nalamula Davide, ndipo anaitentha ndi moto.

13 Ndipo Afilisti anabwerezanso, nafalikira m'cigwamo.

14 Ndipo Davide anafunsiranso kwa Mulungu, nanena Mulungu naye, Usakwera kuwatsata, uwazungulire, nuwadzere pandunji pa mitengo ya mkandankhuku.

15 Ndipo kudzali, pakumva iwe kuwayula kunsonga kwa mitengo ya mkandankhuku, pamenepo uturukire kunkhondo; pakuti Mulungu waturukira pamaso pako kukantha gulu la Afilisti.

16 Nacita Davide monga Yehova adamuuza, nakantha gulu la Afilisti kuyambira ku Gibeoni kufikira ku Gezeri.

17 Ndipo mbiri ya Davide inabuka m'maiko onse, nafikitsira Yehova kuopsa kwace pa amitundu onse.

15

1 Ndipo Davide anadzimangira nyumba m'mudzi mwace, nakonzeratu malo likasa la Mulungu, naliutsira hema.

2 Pamenepo Davide anati, Sayenera ena kusenza likasa la Mulungu koma Alevi ndiwo; pakuti Yehova anawasankha iwo kusenza likasa la Mulungu, ndi kumtumikira iye kosatha.

3 Ndipo Davide anasonkhanitsira Aisrayeli onse ku Yerusalemu, akwere nalo likasa la Yehova kumalo kwace adalikonzera.

4 Ndipo Davide anasonkhanitsa ana a Aroni ndi Alevi;

5 a ana a Kohati, Urieli mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu makumi awiri;

6 a ana a Merari, Adaya mkuru wao, ndi abale ace mazana awiri mphambu makumi awiri;

7 a ana a Gerisomu, Yoeli mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu makumi atatu;

8 a ana a Elizafana, Semaya mkuru wao, ndi abale ace mazana awiri;

9 a ana a Hebroni, Elieli mkuru wao, ndi abale ace makumi asanu ndi atatu;

10 a ana a Uzieli, Aminadabu mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.

11 Ndipo anaitana Zadoki ndi Abyatara ansembe, ndi Alevi Urieli, Asaya, ndi Yoeli, Semaya, ndi Elieli, ndi Aminadabu, nanena nao,

12 Inu ndinu akuru a nyumba za makolo a Alevi, mudzipatule inu ndi abale anu omwe, kuti mukatenge ndi kukwera nalo likasa la Yehova Mulungu wa Israyeli ku malo ndalikonzera.

13 Pakuti, cifukwa ca kusalinyamula inu poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anacita cotipasula, popeza sitinamfunafuma Iye monga mwa ciweruzo.

14 Momwemo ansembe ndi Alevi anadzipatula kuti akwere nalo likasa la Yehova Mulungu wa Israyeli.

15 Ndipo ana a Alevi anasenza likasa la Mulungu pa mapewa ao, mphiko ziri m'mwemo, monga Mose anawauza, monga mwa mau a Yehova.

16 Ndipo Davide ananena ndi mkuru wa Alevi kuti aike abale ao oyimbawo ndi zoyimbira, zisakasa, ndi azeze, ndi nsanje, azimveketse ndi kukweza mau ao ndi cimwemwe.

17 Ndipo Alevi anaika Hemani mwana wa Yoeli, ndi a abale ace Asafu mwana wa Berekiya, ndi a ana a Merari, abale ao, Etani mwana wa Kusaya;

18 ndi pamodzi nao abale ao a kulongosola kwaciwiri, Zekariya, Beni, ndi Yaazieli, ndi Semiramoti, ndi Yehieli, ndi Uni, Bliabu, ndi Benaya, ndi Maaseya, ndi Matitiya, ndi Blifelehu, ndi Mikineya, ndi Obedi Bdomu, ndi Yeieli, ndikirawo.

19 Oyimba tsono: Hemani, Asafu, ndi Btani, anayimba ndi nsanje zamkuwa;

20 ndi Zekariya, ndi Azieli, ndi Semiramod, ndi Yehieli, ndi Uni, ndi Bliabu, ndi Maaseya, ndi Benaya, ndi zisakasa kuyimbira mwa Alimoti;

21 ndi Matitiya, ndi Elifelehu, ndi Mikeya, ndi Obedi Edomu, ndi Yeieli, ndi Azaziya, ndi azeze akuyimbira mwa Seminiti, kutsogolera mayimbidwe.

22 Ndi Kenaniya mkuru wa Alevi anayang'anira kusenzako; anawalangiza za kusenza, pakuti anali waluso.

23 Ndi Berekiya ndi Elikana anali odikira likasa.

24 Ndi Sebaniya, ndi Yosafati, ndi Netaneli, ndi Amasai, ndi Zekariya, ndi Benaya, ndi Eliezere, ansembe, analiza malipenga ku likasa la Mulungu; ndi Obedi Edomu ndi Yehiya anali odikira a likasa.

25 Momwemo Davide, ndi akuru akuru a Israyeli, ndi atsogoleri a zikwi, anamuka kukwera nalo likasa la cipangano la Yehova, kucokera ku nyumba ya Obedi Edomu mokondwera.

26 Ndipo popeza Mulungu anathandiza Alevi akusenza likasa la cipangano la Yehova, iwo anapha nsembe ng'ombe zisanu ndi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri.

27 Ndipo Davide anabvala maraya abafuta, ndi Alevi onse akunyamula likasa, ndi oyimba, ndi Kenaniya woyang'anira kusenzaku, pamodzi ndi oyimba; Davide anabvalanso efodi wabafuta.

28 Momwemo Aisrayeli onse anakwera nalo likasa la cipangano la Yehova ndi kupfuula, ndi kumveka kwa lipenga, ndi mphalasa, ndi nsanje zomveketsa, ndi zisakasa, ndi azeze.

29 Ndipo polowa likasa la cipangano la Yehova m'mudzi wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli anasuzumira pazenera, naona mfumu Davide alikutumphatumpha ndi kusewera; ndipo anampeputsa mumtima mwace.

16

1 Ndipo analowa nalo likasa la Mulungu, nalgka pakati pa hemalo Davide adaliutsira; ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zoyamika pamaso pa Mulungu.

2 Ndipo atatha Davide kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zoyamika, anadalitsa anthu m'dzina la Yehova.

3 Nagwira ali yense wa Israyeli, wamwamuna ndi wamkazi, yense mtanda wa mkate, ndi nthuli ya nyama, ndi ncinci ya mphesa zouma.

4 Ndipo anaika Alevi ena atumikire ku likasa la Yehova, nalalikire, nayamike, nalemekeze Yehova Mulungu wa Israyeli.

5 Asafu ndiye mkuru wao, ndi otsatana naye Zekariya, Yeieli, ndi Semiramoti, ndi Yehieli, ndi Matitiya, ndi Eliabu, ndi Benaya, ndi Obedi Edomu, ndi Yeieli, ndi zisakasa ndi azeze; koma Asafu ndi nsanje zomvekatu;

6 ndi Benaya ndi Yahazieli ansembe ndi malipenga kosalekeza, ku likasa la cipangano la Mulungu.

7 Tsiku limenelo tsono Davide anayamba kuwapatsa nyimbo ya kuyamika nayo Yehova; ocita ndiwo Asafu ndi abale ace.

8 Yamikani Yehova, itanani dzina lace; Bukitsani mwa mitundu ya anthu zocita iye.

9 Myimbireni, myimbireni zomlemekeza; Fotokozerani zodabwiza zace zonse.

10 Mudzitamandire ndi dzina lace lopatulika; Mitima yao ya iwo ofuna Yehova ikondwere.

11 Funsirani kwa Yehova ndi mphamvu yace; Funani nkhope yace nthawi zonse.

12 Kumbukilani zodabwiza zace adazicita, Zizindikilo zace, ndi maweruzo a pakamwa pace;

13 Inu mbeu ya Israyeli mtumiki wace, Inu ana a Yakobo, osankhika ace.

14 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi,

15 Kumbukilani cipangano cace kosatha, Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;

16 Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu, Ndi lumbiro lace ndi Isake;

17 Ndipo anacitsimikizirakwa Yakobo cikhale malemba, Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli;

18 Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani, Gawo la colandira cako;

19 Pokhala inu anthu owerengeka, Inde anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;

20 Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina, Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.

21 Sanalola munthu awasautse; Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;

22 Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga, Musamacitira coipa aneneri anga,

23 Myimbireni Yehova, inu dziko lonse lapansi, Lalikirani cipulumutso cace tsiku ndi tsiku,

24 Fotokozerani ulemerero wace mwa amitundu, Zodabwiza zace mwa mitundu yonse ya anthu.

25 Pakuti Yehova ali wamkuru, nayenera kulemekezedwa kwakukulu; Ayenera amuope koposa milungu yonse.

26 Pakuti milungu ya mitundu ya anthu ndiyo mafano; Koma Yehova analenga zakumwamba.

27 Pamaso pace pali ulemu ndi ukulu, M'malo mwace muli mphamvu ndi cimwemwe.

28 Mcitireni Yehova, inu mafuko a mitundu ya anthu, Mcitireni Yehova ulemerero ndi mphamvu.

29 Mcitireni Yehova ulemerero wa dzina lace; Bwerani naco copereka, ndipo fikani pamaso pace; Lambirani Yehova m'ciyero cokometsetsa,

30 Njenjemerani pamaso pace, inu dziko lonse lapansi, Dziko lokhalamo anthu lomwe lakhazikika, kuti silingagwedezeke.

31 Kukondwerere kumwamba, ndi dziko lapansi lisekerere; Anene mwa amitundu, Yehova acita ufumu.

32 Nyanja ikukume m'kudzala kwace, Munda ukondwerere, ndi zonse ziri m'mwemo;

33 Pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzapfuula mokondwera pamaso pa Yehova; Pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi,

34 Yamikani Yehova; pakuti iye ndiye wabwino; Pakuti cifundo cace ncosatha.

35 Nimunene, Tipulumutseni, Mulungu wa cipulumutso cathu; Mutisokolotse ndi kutilanditsa kwa amitundu, Kuti tiyamike dzina lanu loyera, Ndi kudzitamandira naco cilemekezo canu.

36 Alemekezedwe Yehova Mulungu wa Israyeli, Kuyambira kosayamba kufikira kosatha. Ndipo anthu onse anati, Amen! nalemekeza Yehova.

37 Ndipo anasiyako ku likasa la cipangano la Yehova Asafu ndi abale ace, atumikire kulikasa kosalekeza, monga umo mudzafunika tsiku ndi tsiku;

38 ndi Obedi Edomu, ndi abale ace makumi asanu ndi limodzi mphambu asanu ndi atatu; ndi Obedi Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa akhale odikira;

39 ndi Zadoki wansembe, ndi abale ace ansembe, ku kacisi wa Yehova, pa msanje unali ku Gibeoni;

40 kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa la nsembe zopsereza, kosalekeza, m'mawa ndi madzulo, monga mwa zonse zilembedwa m'cilamulo ca Yehova adacilamulira Israyeli;

41 ndi pamodzi nao Hemani, ndi Yedutuni, ndi osankhika otsalawo, ochulidwa maina, kuyamika Yehova; pakuti cifundo cace ncosatha;

42 ndi pamodzi nao Hemani, ndi Yedutuni, ndi malipenga ndi nsanje za iwo akumveketsadi, ndi zoyimbira nyimbo za Mulungu; ndi ana a Yedutuni anakhala kucipata.

43 Ndipo anacoka anthu onse, yense ku nyumba yace, nabwera Davide kudalitsa nyumba yace.

17

1 Ndipo pokhala Davide m'nyumba mwace, Davideyo anati kwa Natani mneneri, Taona, ndikhala ine m'nyumba yamikungudza, koma Gkasa la cipangano likhala m'nsaru zocinga.

2 Ndipo Natani anati kwa Davide, Mucite zonse ziri m'mtima mwanu; pakuti Mulungu ali nanu.

3 Ndipo usiku womwewo mau a Mulungu anadzera Natani, ndi kuti,

4 Kauze Davide mtumiki wanga, Atero Yehova, Usandimangire nyumba yokhalamo;

5 pakuti sindinakhala m'nyumba kuyambira tsiku tija ndinakwera naye Israyeli, kufikira lero Gno; koma wa m'hema m'hema Ine, ndi wa m'kacisi m'kacisi,

6 Pali ponse ndinayenda nao Aisrayeli onse ndinanena kodi mau ndi woweruza ali yense wa Israyeli, amene ndinamuuza adyetse anthu anga, ndi kuti, Mwalekeranji kundimangira nyumba yamikungudza?

7 Cifukwa cace tsono, uzitero naye mtumiki wanga Davide, Atero Ambuye wa makamu, Ndinakutenga kubusa potsata iwe nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Israyeli;

8 ndipo ndakhala ndi iwe kuli konse unamukako, ndi kuononga adani ako onse pamaso pako; ndipo ndakubukitsira dzina lakunga dzina la akuru okhala padziko.

9 Ndipo ndaikira anthu anga Israyeli malo, ndi kuwaoka, kuti akhale m'malo mwao osasunthikanso; ndi ana osalungama sadzawapululanso monga poyamba paja;

10 ndi kuyambira kuja ndinaika oweruza ayang'anire anthu anga Israyeli; ndipo ndagonjetsa adani ako onse. Ndikuuzanso kuti Yehova adzakumangira banja.

11 Ndipo kudzacitika, atakwanira masiku ako kuti uzipita kukhala ndi makolo ako, ndidzaukitsa mbeu yako pambuyo pako, ndiye wa ana ako; ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wace.

12 Iye adzandimangira nyumba; ndipo ndidzakhazikitsa mpando wacifumu wace kosatha.

13 Ndidzakhala atate wace, ndi iye adzakhala mwana wanga; ndipo sindidzamcotsera cifundo canga monga muja ndinacotsera iye amene anakhala usanakhale iwe;

14 koma ndidzamkhazikitsa m'nyumba mwanga, ndi m'ufumu wanga kosatha; ndi mpando wa cifumu wace udzakhazikika kosatha.

15 Monga mwa mau awa onse, ndi monga mwa masomphenya awa onse, momwemo Natani analankhula ndi Davide.

16 Pamenepo mfumu Davide analowa nakhala pamaso pa Yehova, nati, Ndine yani, Yehova Mulungu, ndi nyumba yanga njotani kuti mwandifikitsa mpaka pano?

17 Ndipo ici ncacing'ono pamaso panu, Mulungu, koma mwanena za nyumba ya mtumiki wanu nthawi yam'tsogolo ndithu, ndipo mwandiyesera ngati munthu womveka, Yehova Mulungu.

18 Anenenjinso Davide kwa Inu za ulemu wocitikira mtumiki wanu? pakuti mudziwa mtumiki wanu.

19 Yehova, cifukwa ca mtumiki wanu, ndi monga mwa mtima wanu, mwacita ukulu uwu wonse, kundidziwitsa zazikuru izi zonse.

20 Yehova, palibe wina wonga inu, palibenso Mulungu wina koma Inu; monga mwa zonse tazimva m'makutu mwathu.

21 Ndiwo ayani akunga anthu anu Israyeli, mtundu wa pa wokha wa pa dziko lapansi, amene Mulungu anakadziombolera mtundu wa anthu, kudzibukitsira dzina, mwa zazikuru ndi zoopsa, pakupitikitsa amitundu pamaso pa anthu anu amene munawaombola m'Aigupto?

22 Pakuti anthu anu Israyeli mudawayesa anthu anu anu kosatha; ndipo Inu, Yehova, munayamba kukhala Mulungu wao.

23 Ndipo tsopano, Yehova, akhazikike kosalekeza mau mudanenawa za mtumiki wanu, ndi za nyumba yace, nimucite monga mwanena.

24 Inde likhazikike dzina lanu, likulitsidwe kosalekeza, ndi kuti, Yehova wa makamu ndiye Mulungu wa Israyeli; akhalira Israyeli Mulungu; ndi nyumba ya Davide mtumiki wanu ikhazikika pamaso panu.

25 Pakuti Inu, Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzammangira banja; momwemo mtumiki wanu waona mtima wakupemphera pamaso panu.

26 Ndipo tsopano, Yehova, Inu ndinu Mulungu, ndipo mwanenera mtumiki wanu cokoma ici;

27 cakukomerani kudalitsa nyumba ya mtumiki wanu, kuti ikhalebe kosatha pamaso panu; pakuti Inu Yehova mwadalitsa, ndipo idzadalitsika kosatha.

18

1 Ndipo zitatha izi, Davide anakantha Afilisti, nawagonjetsa, nalanda Gati ndi midzi yace m'manja a Afilisti.

2 Anakanthanso Moabu; ndi Amoabu anakhala anthu a Davide, nabwera nazo mphatso,

3 Ndipo Davide anakantha Hadarezeri mfumu ya Zoba ku Hamati, pomuka iye kukhazikitsa ulamuliro wace ku mtsinje wa Firate.

4 Ndipo Davide analanda magareta ace cikwi cimodzi, ndi apakavalo zikwi zisanu ndi ziwiri, ndi oyenda pansi zikwi makumi awiri; Davide anadula mitsita akavalo onse okoka magareta, koma anasungako ofikira magareta zana limodzi.

5 Ndipo Aaramu a ku Damasiko anadza kudzathandiza Hadarezeri mfumu ya Zoba; koma Davide anakantha Aaramu amuna zikwi makumi awiri mphambu ziwiri.

6 Ndipo Davide anaika asilikari a boma m'Aramu wa Damasiko; ndi Aaramu anasanduka anthu a Davide, nabwera nazo mphatso, Ndipo Yehova anasunga Davide kuli konse anamukako.

7 Natenga Davide zikopa zagolidi zinali pa anyamata a Hadarezeri, nabwera nazo ku Yerusalemu.

8 Ndi ku Tibati, ndi ku Kuni, midzi ya Hadarezeri, Davide anatenga mkuwa wambiri, ndiwo umene Solomo anayenga nao thawale lamkuwa, ndi nsanamira, ndi zipangizo zamkuwa.

9 Ndipo pakumva Tou, mfumu ya ku Hamati, kuti Davide adakantha khamu lonse la Hadarezeri mfumu ya ku Zoba,

10 anatumiza Hadoramu mwana wace kwa Davide, kumlankhula ndi kumdalitsa, popeza adayambana ndi Hadarezeri, namkantha; pakuti Hadarezeri adacita nkhondo ndi Tou; ndipo anali nazo zipangizo za mitundu mitundu za golidi ndi siliva ndi mkuwa.

11 Izi zomwe mfumu Davide anazipatulira Yehova, pamodzi ndi siliva ndi golidi adazitenga kwa amitundu onse, kwa Edomu, ndi kwa Moabu, ndi kwa ana a Amoni, ndi kwa Afilisti, ndi kwa Amaleki.

12 Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu m'Cigwa ca Mcere zikwi khumi mphambu zisanu ndi zitatu.

13 Ndipo anaika asilikari a boma m'Edomu; ndi Aedomu onse anasanduka anthu a Davide. Ndipo Yehova anasunga Davide kuli konse anamukako.

14 Ndipo Davide anakhala mfumu ya Aisrayeli onse, naweruza anthu ace onse, nawacitira cilungamo.

15 Ndipo Yoabu mwana wa Zeruya anayang'anira khamu la nkhondo, ndi Yehosafati mwana wa Ahiludi anali wolemba mbiri.

16 Ndi Zadoki mwana wa Ahitubu, ndi Abimeleki mwana wa Abyatara, anali ansembe, ndi Savisa anali mlembi,

17 ndi Benaya mwana wa Yehoyada anayang'anira Akereti ndi Apeleti; koma ana a Davide ndiwo oyamba ku dzanja la mfumu.

19

1 Ndipo zitatha izi, Nahasi mfumu ya ana a Amoni anamwalira, ndi mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

2 Ndipo Davide anati, Ndidzamcitira zokoma mtima Hanuni mwana wa Nahasi, popeza atate wace anandicitira ine zokoma mtima. Momwemo Davide anatuma mithenga imtonthoze mtima pa atate wace. Pofika anyamata ace a Davide ku dziko la ana a Amoni kwa Hanuni kumtonthoza mtima,

3 akalonga a ana a Amoni anati kwa Hanuni, Davide ali kucitira atate wanu ulemu kodi, popeza anakutumizirani otonthoza? sakudzerani kodi anyamata ace kufunafuna, ndi kugubuduza, ndi kuzonda dziko?

4 Ndipo Hanuni anatenga anyamata a Davide, nawameta, nadula malaya ao pakati kufikira m'matako, nawaleka acoke.

5 Pamenepo anamuka ena, namuuza Davide za amunawa. Natumiza iye kukomana nao, pakuti amunawa anacita manyazi kwambiri. Ndipo mfumu inati, Balindani ku Yeriko mpaka zamera ndebvu zanu; zitamera mubwere.

6 Ndipo pamene ana a Amoni anaona kuti anadzinunkhitsa kwa Davide, Hanuni ndi ana a Amoni anatumiza matalente cikwi cimodzi a siliva, kudzilembera magareta ndi apakavalo ku Mesopotamiya, ndi ku Aramu-maaka, ndi ku Zoba.

7 Momwemo anadzilembera magareta zikwi makumi atatu mphambu ziwiri, ndi mfumu ya Maaka ndi anthu ace; nadza iwo, namanga misasa cakuno ca Medeba. Ana a Amoni omwe anasonkhana m'midzi mwao, nadza kunkhondo.

8 Pamene Davide anamva ici anatuma Yoabu ndi gulu lonse la anthu amphamvu.

9 Ndipo ana a Amoni anaturuka, nandandalitsa nkhondo ku cipata ca mudzi, ndi mafumu adadzawo anali pa okha kuthengo.

10 Pakuona Yoabu tsono kuti nkhondo inamdzera kumaso ndi kumbuyo, anasankha amuna osankhika onse a Israyeli, nawanika ayambane ndi Aaramu.

11 Ndipo anthu otsala anawapereka m'dzanja la Abisai mbale wace; ndipo anadzinika avambane ndi ana a Amoni.

12 Ndipo anati, Akandilaka Aaramu, udzandilanditsa ndiwe; koma akakulaka ana a Amoni, ndidzakulanditsa ndine.

13 Limbika mtima, tilimbikire anthu athu, ndi midzi ya Mulungu wathu; ndipo Yehova acite comkomera.

14 Pamenepo Yoabu ndi anthu anali naye anayandikira pamaso pa Aaramu kulimbana nao, ndipo anawathawa.

15 Ndipo pakuona ana a Amoni kuti adathawa Aaramu, iwo omwe anathawa pamaso pa Abisai mbale wace, nalowa m'mudzi. Pamenepo Yoabu anadza ku Yerusalemu.

16 Ndipo pakuona Aaramu kuti Israyeli anawakantha, anatumiza mithenga, naturuka nao Aaramu akukhala tsidya lija la mtsinjewo; ndi Sofaki kazembe wa khamu la Hadarezeri anawatsogolera.

17 Ndipo anamuuza Davide; namemeza iye Aisrayeli onse, naoloka Yordano, nawadzera, nanika nkhondo ayambane nao. Atandandalitsa nkhondo Davide kuyambana ndi Aaramu, anaponyana naye.

18 Ndipo Aaramu anathawa pamaso pa Israyeli; ndipo Davide anapha Aaramu apamagareta zikwi zisanu ndi ziwiri, ndi oyenda pansi zikwi makumi anai; napha Sofaki kazembe wa khamulo.

19 Ndipo pakuona anyamata a Hadarezeri kuti Israyeli anawakantha, anapangana mtendere ndi Davide, namtumikira; ndi Aaramu anakana kuthandizanso ana a Amoni.

20

1 Ndipo kunali, pofikanso caka, nyengo yakuturuka mafumu, Yoabu anatsogolera khamu lamphamvu, napasula dziko la ana a Amoni, nadza, naumangira misasa Raba. Koma Davide anakhala ku Yerusalemu. Ndipo Yoabu anakantha Raba, naupasula.

2 Ndipo Davide anatenga korona wa mfumu yao kumcotsa pamutu pace, napeza kulemera kwace talente wa golidi; panalinso miyala ya mtengo wace pamenepo; ndipo anamuika pamutu pa Davide, naturutsa zankhondo za m'mudzimo zambiri ndithu.

3 Naturutsanso anthu anali m'mwemo, nawaceka ndi mipeni ya mana mano, ndi zipangizo zocekera zacitsulo, ndi nkhwangwa. Anatero Davide ndi midzi yonse ya ana a Amoni. Ndipo Davide ndi anthu onse anabwera ku Yerusalemu.

4 Ndipo zitatha izi, inauka nkhondo ku Gezeri ndi Afilisti; pamenepo Sibekai Mhusati anapha Sipai wa ana a cimphona; ndipo anawagonjetsa.

5 Ndipo panalinso nkhondo ndi Afgisti; ndi Elihanani mwana wa Yairi anapha Lami mbale wa Goliati Mgiti, amene luti la mkondo wace linanga mtanda woombera nsaru.

6 Ndipo panalinso nkhondo ku Gati; kumeneko kunali munthu wa msinkhu waukuru, amene zala zace za kumanja ndi kumapazi ndizo makumi awiri mphambu zinai; zisanu ndi cimodzi ku dzanja liri lonse, ndi zisanu ndi cimodzi ku phazi liri lonse; nayenso anabadwa mwa cimphonaco.

7 Ndipo potonza Israyeli iyeyu Yonatani mwana wa Simeya mbale wace wa Davide anamkantha.

8 Awa anabadwa mwa cimphonaco ku Gati, koma anagwa ndi dzanja la Davide ndi la anyamata ace.

21

1 Pamenepo Satana anaukira Israyeli, nasonkhezera Davide awerenge Israyeli.

2 Ndipo Davide anati kwa Yoabu ndi kwa akuru a anthu, Kawerengeni Israyeli kuyambira ku Beereseba kufikira ku Dani; nimundibwezere mau, kuti ndidziwe ciwerengo cao.

3 Nati Yoabu, Yehova aonjezere pa anthu ace monga ali kazana; koma, mbuyanga mfumu, sali onse anyamata akapolo a mbuyanga? nanga afuniranji cinthuci mbuyanga, adzaparamulitsa Israyeli bwanji?

4 Koma mau a mfumu anamlaka Yoabu. Naturuka Yoabu, nakayendayenda mwa Aisrayeli onse, nadza ku Yerusalemu.

5 Ndipo Yoabu anapereka kwa Davide ciwerengo ca anthu owerengedwa. Ndipo Aisrayeli onse anali zikwi mazana khumi ndi limodzi osolola lupanga, ndi Yuda anali zikwi mazana anai mphambu makumi asanu ndi awiri akusolola lupanga,

6 Koma sanawerenga Alevi ndi Abenjamini pakati pao; pakuti mau a mfumu anamnyansira Yoabu.

7 Ndipo Mulungu anaipidwa naco cinthuci, cifukwa cace iye anakantha Israyeli.

8 Pamenepo Davide anati kwa Mulungu, Ndacimwa kwakukuru ndi kucita cinthu ici; koma tsopano, mucotse mphulupulu ya kapolo wanu, pakuti ndacita kopusa ndithu.

9 Ndipo Yehova ananena ndi Gadi mlauli wa Davide, ndi kuti,

10 Kanene kwa Davide kuti, Atero Yehova, Ndikuikira zitatu; dzisankhireko cimodzi ndikucitire ici.

11 Nadza Gadi kwa Davide, nanena naye, Atero Yehova, Dzitengereko;

12 kapena zaka zitatu za njala; kapena miyezi itatu ya kuthedwa pamaso pa adani ako, ndi kuti lupanga la adani ako likupeze; kapena masiku atatu lupanga la Yehova, ndilo mliri m'dzikomo, ndi mthenga wakuononga wa Yehova mwa malire onse a Israyeli, Ulingirire tsono, ndimbwezere mau anji iye amene anandituma ine?

13 Ndipo Davide anati kwa Gadi, Ndipsinjika kwambiri; ndigwere m'dzanja la Yehova, pakuti zifundo zace zicurukadi; koma ndisagwere m'dzanja la munthu.

14 Momwemo Yehova anatumiza mliri pa Israyeli; ndipo adagwapo amuna zikwi makumi asanu ndi awiri a Israyeli.

15 Ndipo Mulungu anatuma mthenga ku Yerusalemu kuuononga; ndipo poti auononge, Yehova anapenya, naleka coipaci; nati kwa mthenga wakuononga, Cakwanira, bweza dzanja lako tsopano. Ndi mthenga wa Yehova anaima pa dwale la Orinani Myebusi,

16 Ndipo Davide anakweza maso ace, naona mthenga wa Yehova alikuima pakati pa dziko ndi thambo, ali nalo lupanga losolola m'dzanja lace, lotambasukira pa Yerusalemu. Pamenepo Davide ndi akuru obvala ziguduli anagwa nkhope zao pansi.

17 Ndipo Davide anati kwa Mulungu, Si ndine nanga ndalamulira kuti awerenge anthu? Inde, ndine amene ndacimwa ndi kucita coipa ndithu; koma nkhosa izi zinacitanji? dzanja lanu, Yehova Mulungu wanga, Gnditsutse ine ndi nyumba ya atate wanga, koma Gsatsutse anthu anu ndi kuwacitira mliri.

18 Pamenepo mthenga wa Yehova anauza Gadi kuti anene ndi Davide, akwere Davideyo kuutsira Yehova guwa la nsembe pa dwale la Orinani Myebusi,

19 Ndipo Davide anakwera monga mwa mau a Gadi adawanena m'dzina la Yehova.

20 Poceuka Orinani anaona wamthengayo; ndi ana ace amuna anai anali naye anabisala. Koma Orinani analikupuntha tirigu.

21 Ndipo pofika Davide kwa Orinani, Orinaniyo anapenyetsa, naona Davide, naturuka kudwale, nawerama kwa Davide, nkhope yace pansi.

22 Davide tsono anati kwa Orinani, Ndipatse padwale pano kuti ndimangepo guwa la nsembe la Yehova; undipatse gi pa mtengo wace wonse, kuti mliri ulekeke pa anthu.

23 Ndipo Orinani anati kwa Davide, Mulitenge, ndi mbuye wanga mfumu icite comkomera m'maso mwace; taonani, ndikupatsani ng'ombe za nsembe zopsereza; ndi zipangizo zopunthira zikhale nkhuni, ndi tirigu wa nsembe yaufa; ndizipereka zonse.

24 Koma mfumu Davide anati kwa Orinani, lai, koma ndidzaligula pa mtengo wace wonse; pakuti sindidzatengera Yehova ciri cako, kapena kupereka nsembe yopsereza yopanda mtengo wace.

25 Momwemo Davide anapatsa Orinani cogulira malowa golidi wa masekeli mazana asanu ndi limodzi kulemera kwace.

26 Ndipo Davide anamangira Yehova guwa la nsembe komweko; napereka nsembe zopsereza, ndi nsembe zoyamika, naitana kwa Yehova; ndipo anamyankha ali m'Mwamba ndi mota pa guwa la nsembe yopsereza.

27 Ndipo Yehova anauza wamthenga kuti abweze lupanga lace m'cimace.

28 Nthawi yomweyi, pakuona Davide kuti Yehova anambvomereza pa dwale la Orinani Myebusi, anaphera nsembe pomwepo.

29 Pakuti kacisi wa Yehova amene Mose anapanga m'cipululu, ndi guwa la nsembe yopsereza, zinali pa msanje wa ku Gibeoni nthawi yomweyi.

30 Kama Davide sanathe kumuka kukhomo kwace kufunsira kwa Mulungu, pakuti anaopa lupanga la mthenga wa Yehova.

22

1 Ndipo Davide anati, Pano padzakhala nyumba ya Yehova Mulungu, ndi pano padzakhala guwa la nsembe yopsereza la Israyeli.

2 Ndipo Davide anati asonkhanitse alendo okhala m'dziko la Israyeli; iye naika osema miyala afukule miyala, aiseme kuti amange nayo nyumba ya Mulungu.

3 Nakonzeratu Davide citsulo cocuruka ca misomali ya ku zitseko za zipata, ndi ya kuphatikizitsa; ndi mkuwa wocuruka wosauyesa kulemera kwace;

4 ndi mitengo yamikungudza yosaiwerenga; pakuti Asidoni ndi Aturo anabwera nayo kwa Davide mitengo yamikungudza yocuruka,

5 Ndipo Davide anati, Solomo mwana wanga ndiye mnyamata ndi wosakwima, ndi nyumba imene adzaimangira Yehova ikhale yaikuru yopambana, yomveka ndi ya ulemerero mwa maiko onse; ndiikonzeretu mirimo. Momwemo Davide anakonzeratu mocuruka asanamwalire.

6 Pamenepo iye anaitana Solomo mwana wace, namlangiza ammangire Yehova Mulungu wa Israyeli nyumba.

7 Ndipo Davide anati kwa Solomo mwana wace, Kunena za ine, kumtima kwanga kudati, ndilimangire dzina la Yehova Mulungu wanga nyumba.

8 Koma mau a Yehova anandidzera, kuti, Wakhetsa mwazi wocuruka, popeza wacita nkhondo zazikuru; sudzamangira dzina langa nyumba, popeza wakhetsa pansi mwazi wambiri pamaso panga;

9 taona, udzabala mwana, ndiye adzakhala munthu wa phe; ndipo nelidzampumulitsira adani ace onse pozungulirapo, pakuti dzina lace lidzakhala Solomo; ndipo ndidzapatsa Israyeli mtendere ndi bata masiku ace;

10 iyeyu adzamangira dzina langa nyumba; iye adzakhala mwana wanga, ndi Ine ndidzakhala Atate wace; ndipo ndidzakhazikitsa mpando wacifumu wa ufumu wace pa Israyeli kosalekeza.

11 Tsono, mwana wanga, Yehova akhale nawe; nulemerere, numange nyumba ya Yehova Mulungu wako monga ananena za iwe.

12 Cokhaci, Yehova akupatse nzeru ndi luntha, nakulangize za Israyeli, kuti usunge cilamulo ca Yehova Mulungu wako,

13 Momwemo udzalemerera, ukasamalira kucita malemba ndi maweruzo amene Yehova analangiza Mose za Israyeli; limbikatu, nulimbike mtima, usaope, usade mtima.

14 Taona tsono, m'kuzunzika kwanga ndinakonzeratu nyumba ya Yehova matalente zikwi zana limodzi a golidi, ndi matalente zikwi zikwi a siliva, ndi mkuwa, ndi citsulo, osayesa kulemera kwace, pakuti zidacurukaeli; mitengo yomwe ndi miyala ndakonzeratu; nuonjezereko.

15 Uli naonso anchito ocuruka ofukula miyala, ndi amisiri a miyala ndi a mitengo, ndi amuna onse aluso akucita nchito ziri zonse;

16 golidi, ndi siliva, ndi mkuwa, ndi citsulo, nzosawerengeka; nyamuka, nucite, Yehova akhale nawe.

17 Davide analangizanso akalonga a Israyeli athanelize Solomo mwana wace, ndi kuti,

18 Kodi Yehova Mulungu wanu sali nanu? sanakupumulitsani pambali ponse? pakuti anapereka nzika za m'dziko m'dzanja mwanga, ndi dziko lagonjetsedwa pamaso pa Yehova, ndi pamaso pa anthu ace.

19 Perekani tsono mtima ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu; ndipo nyamukani ndi kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti abwere nalo likasa la cipangano la Yehova, ndi zipangizo zopatulika za Mulungu, ku nyumba imene idzamangidwira dzina la Yehova.

23

1 Atakalamba tsono Davide ndi kucuruka masiku, iye analonga mwana wace Solomo akhale mfumu ya Israyeli.

2 Ndipo anasonkhanitsa akuru onse a Israyeli, ndi ansembe ndi Alevi.

3 Ndipo anawerengedwa Alevi oyambira zaka makumi atatu ndi mphambu, ndipo ciwerengo cao kuwawerenga mmodzi mmodzi ndico amuna zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu.

4 A iwowa zikwi makumi awiri mphambu zinai anayang'anira nchito ya nyumba ya Yehova, ndi zikwi zisanu ndi cimodzi ndiwo akapitao ndi oweruza,

5 ndi zikwi zinai odikira; ndi zikwi zinai analemekeza Yehova ndi zoyimbira zimene ndinazipanga, anati Davide, kuti alemekeze nazo.

6 Ndipo Davide anawagawa magawo monga mwa ana a Levi: Gerisomu, Kohati, ndi Merari.

7 A Agerisomu: Ladani ndi Simeyi,

8 Ana a Ladani: wamkuru ndi Yehieli, ndi Zethamu, ndi Yoeli; atatu.

9 Ana a Simeyi: Selomoti, ndi Hazieli, ndi Hanani; atatu. Ndiwo akuru a nyumba za makolo a Ladani.

10 Ndi ana a Simeyi: Yahati, Zina, ndi Yeusi, ndi Beriya. Awa anai ndiwo ana a Simeyi.

11 Wamkuru wa iwo ndi Yahati, mnzace ndi Ziza; koma Yeusi ndi Beriya analibe ana ambiri, potero anakhala nyumba ya kholo yowerengedwa pamodzi.

12 Ana a Kohati: Amiramu, Izara, Hebroni, ndi Uzieli; anai.

13 Ana a Amiramu: Aroni, ndi Mose; ndipo Aroni anasankhidwa kuti apatule zopatulikitsa, iye ndi ana ace, kosalekeza, kufukiza pamaso pa Yehova, kumtumikira, ndi kudalitsa m'dzina lace kosatha.

14 Kunena za Mose munthu wa Mulunguyo, ana ace anaehulidwa mwa pfuko la Levi.

15 Ana a Mose: Gerisomu, ndi Eliezeri.

16 Ana a Gerisomu: wamkuru ndi Sebuyeli.

17 Ndi ana a Eliezeri: wamkuru ndi Rehabiya. Ndipo Eliezeri analibe ana ena, koma ana a Rehabiya anacuruka kwambiri.

18 Ana a Izara: wamkuru ndiye Selomiti.

19 Ana a Hebroni: wamkuru ndi Yeriya, waciwiri ndi Amariya, wacitatu ndi Yehazieli, wacinai ndi Yekameamu,

20 Ana a Uzieli: wamkuru ndi Mika, waciwiri ndi Isiya.

21 Ana a Merari: Mali ndi Musi. Ndi ana a Mali: Eleazara ndi Kisi.

22 Nafa Eleazara wopanda ana amuna, koma ana akazi ndiwo; ndi asuweni ao ana a Kisi anawatenga akhale akazi ao.

23 Ana a Musi: Mali, ndi Ederi, ndi Yeremoti; atatu.

24 Awa ndi ana a Levi monga mwa nyumba za makolo ao, ndiwo akuru a nyumba za makolo a iwo owerengedwa mwa ciwerengo ca maina mmodzi mmodzi, akugwira nchito ya utumiki wa nyumba ya Yehova, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu.

25 Pakuti Davide anati, Yehova Mulungu wa Israyeli wapumulitsa anthu ace; ndipo akhala m'Yerusalemu kosatha;

26 ndiponso Alevi asasenzenso kacisi ndi zipangizo zace zonse za utumiki wace.

27 Pakuti monga mwa mau ace otsiriza a Davide, ana a Levi anawerengedwa kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu.

28 Pakuti nchito yao ndiyo kuimirira ana a Aroni, atumikire m'nyumba ya Yehova, m'mabwalo, ndi kuzipinda, ndi kuyeretsa zopatulika zonse; inde nchito za utumiki wa nyumba ya Mulungu;

29 ya mkate woonekera womwe, ndi ya ufa wosalala wa nsembe yaufa, ndi ya timitanda taphanthiphanthi topanda cotupitsa, ndi ya ciwaya, ndi yakukazinga, ndi ya miyeso iri yonse;

30 ndi kuimirira m'mawa ndi m'mawa kuyamika ndi kulemekeza Yehova, momwemonso madzulo;

31 ndi kupereka nsembe zopsereza zonse kwa Yehova, za masabata, za pokhala mwezi, za nyengo zoikika, kuwerenga kwace monga mwa lemba lace, kosalekeza pamaso pa Yehova;

32 ndi kuti asunge udikiro wa cihema cokomanako, ndi udikiro wa malo opatulika ndi udikiro wa ana a Aroni abale ao, potumikira nyumba ya Yehova.

24

1 Ndipo magawidwe a ana a Aroni ndi awa. Ana a Aroni: Nadabu, ndi Abihu, Eleazara, ndi Itamara.

2 Koma Nadabu ndi Abihu anafa, atate wao akali ndi moyo, opanda ana; momwemo Eleazara ndi ltamara anacita nchito ya nsembe.

3 Ndipo Davide pamodzi ndi Zadoki wa ana a Eleazara, ndi Ahimeleke wa ana a Itamara, anawagawa, monga mwa malongosoledwe ao m'utumiki wao.

4 Ndipo anapeza kuti amuna akuru a ana a Eleazara anacuruka, a ana a Itamara anacepa; nawagawa motero: pa ana a Eleazara panali khumi mphambu asanu ndi mmodzi, akuru a nyumba za makolo; ndi pa ana a Itamara, monga mwa nyumba za makolo ao, panali asanu ndi atatu.

5 Ndipo anawagawa ndi maere, awa ndi aja; pakuti panali akalonga a malo opatulika, ndi akalonga a kwa Mulungu, a ana a Eleazara ndi a ana a Itamara omwe.

6 Ndi Semaya mwana wa Netaneli mlembi, ndiye wa Alevi, anawalembera pamaso pa mfumu; ndi akalonga, ndi Zadoki wansembe, ndi Ahimeleke mwana wa Abyatara, a akuru a nyumba za makolo a ansembe ndi Alevi, anatenga nyumba imodzi ya kholo lace ya Eleazara, ndi imodzi ya Itamara.

7 Ndipo maere oyamba anamgwera Yehoyaribu, waciwiri Yedaya,

8 wacitatu Harimu, wacinai Seorimu,

9 wacisanu Malikiya, wacisanu ndi cimodzi Miyamini,

10 wacisanu ndi ciwiri Hakozi, wacisanu ndi citatu Abiya,

11 wacisanu ndi cinai Yesuwa, wakhumi Sekaniya,

12 wakhumi ndi cimodzi Eliyasibu, wakhumi ndi ciwiri Yakimu,

13 wakhumi ndi citatu Hupa, wakhumi ndi cinai Yesebeabu,

14 wakhumi ndi cisanu Biliga, wakhumi ndi cisanu ndi cimodzi Imeri,

15 wakhumi ndi cisanu ndi ciwiri Heziri, wakhumi ndi cisanu ndi citatu Hapizezi,

16 wakhumi ndi cisanu ndi cinai Petahiya, wa makumi awiri Yehezikeli,

17 wa makumi awiri ndi cimodzi Yakini, wa makumi awiri ndi ciwiri Gamuli,

18 wa makumi awiri ndi citatu Delaya, wa makumi awiri ndi cinai Miziya.

19 Awa ndi malongosoledwe ao m'utumiki wao kulowa m'nyumba ya Yehova, monga mwa ciweruzo adawapatsa Aroni atate wao, monga Yehova Mulungu wa Israyeli anamlamulira.

20 Ndipo wa ana otsala a Levi: wa ana a Amiramu, Subaeli; wa ana a Subaeli, Yedeya.

21 Wa Rehabiya: wa ana a Rehabiya, mkuru ndi Isiya.

22 Wa Aizari: Selomoti; wa ana a Selomoti, Yahati.

23 Ndi wa ana a Hebroni: mkuru ndi Yeriya, waciwiri Amariya, wacitatu Yahazieli, wacinai Yekameamu.

24 Wa ana a Uziyeli, Mika; wa ana a Mika, Samiri.

25 Mbale wa Mika, Isiya; a ana a Isiya, Zekariya,

26 Ana a Merari: Mali ndi Musi; mwana wa Yaziya, Beno.

27 Ana a Merari: wa Yaziya, Beno, ndi Sohamu, ndi Sakuri, ndi Ibri.

28 Wa Mali: Eleazara, ndiye wopanda ana.

29 Wa Kisi: mwana wa Kisi, Yerameli.

30 Ndi ana a Musi: Mali, ndi Ederi, ndi Yerimoti, Awa ndi ana a Alevi monga mwa nyumba za makolo ao.

31 Awanso anacita maere monga abale ao ana a Aroni, pamaso pa Davide mfumu, ndi Zadoki, ndi Ahimeleki, ndi akuru a nyumba za makolo za ansembe ndi Alevi; mkuru wa nyumba za makolo monga mng'ono wace.

25

1 Ndipo Davide ndi akazembe a gulu la nkhondo anapatulira utumikiwo ena a ana a Asafu, ndi a Hemani, ndi a Yedutuni, anenere ndi azeze, ndi zisakasa, ndi nsanje; ndi ciwerengo ca anchito monga mwa kutumikira kwao ndko:

2 a ana a Asafu: Zakuri, ndi Yosefe, ndi Netaniya, ndi Asarela, ana a Asafu; mwa cilangizo ca Asafu, wakunenera mwa cilangizo ca mfumu.

3 A Yedntuni, ana a Yedutuni: Gedaliya, ndi Zeri, ndi Yesaya, Hasabiya, ndi Matitiya, asanu ndi mmodzi; mwa cilangizo ca atate wao Yedutuni, ndiye wakunenera ndi kuyamika ndi kulemekeza Yehova ndi zeze.

4 A Hemani, ana a Hemani: Bukiya, Mataniya, Uziyeli, Sebuyeli, ndi Yerimoti, Hananiya, Hanani, Eliyata, Gidaliti, ndi Romamti-Ezeri, Yosibekasa, Maloti, Hotiri, Mahazioti;

5 awa onse ndiwo ana a Hemani mlauli wa mfumu m'mau a Mulungu, kuti akweze mphamvu yace. Ndipo Mulungu anapatsa Hemani ana amuna khumi ndi anai, ndi ana akazi atatu.

6 Onsewa anawalangiza ndi atate wao ayimbe m'nyumba ya Yehova ndi nsanje, zisakasa ndi azeze; atumikire nazo m'nyumba ya Mulungu; ndipo Asafu, Yedutuni, ndi Hemani, anawalangiza ndi mfumu.

7 Ndipo ciwerengo cao, pamodzi ndi abale ao ophunzitsidwa ayimbire Yehova, onse anthetemya, ndiwo mazana awiri mphambu makumi asanu ndi atatu.

8 Ndipo anacita maere pa udikiro wao, analingana onse, ang'ono ndi akuru, mphunzitsi ndi wophunzira.

9 Maere oyamba tsono anagwera a banja la Asafu ndiye Yosefe; waciwiri Gedaliya, iye ndi abale ace, ndi ana ace khumi ndi awiri;

10 wacitatu Zakuri, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

11 wacinai Izri, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

12 wacisanu Netaniya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

13 wacisanu ndi cimodzi Bukiya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

14 wacisanu ndi ciwiri Yesarela: ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

15 wacisanu ndi citatu Yesaya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

16 wacisanu ndi cinai Mataniya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri:

17 wakhumi Simeyi, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

18 wakhumi ndi cimodzi Azareli, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

19 wakhumi ndi ciwiri Hasabiya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

20 wakhumi ndi citatu Subaeli, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

21 wakhumi ndi cinai Matitiya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

22 wakhumi ndi cisanu Yeremoti, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

23 wakhumi ndi cisanu ndi cimodzi Hananiya, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

24 wakhumi ndi cisanu ndi ciwiri Yosibekasa, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

25 wakhumi ndi cisanu ndi citatu Hanani, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

26 wakhumi ndi cisanu ndi cinai Maloti, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

27 wa makumi awiri Eliyata, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

28 wa makumi awiri ndi cimodzi Hotiri, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

29 wa makumi awiri ndi ciwiri Gidaliti, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

30 wa makumi awiri ndi citatu Mahazioti, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri;

31 wa makumi awiri ndi cinai RomamtiEzeri, ana ace ndi abale ace khumi ndi awiri.

26

1 A magawidwe a odikira a Akora: Meselemiya mwana wa Kore wa ana a Asafu.

2 Ndipo Meselemiya anali ndi ana, woyamba Zekariya, waciwiri Yedyaeli, wacitatu Zebadiya, wacinai Yatiniyeli,

3 wacisanu Elamu, wacisanu ndi cimodzi Yohanana, wacisanu ndi ciwiri Elihunai.

4 Ndipo Obedi Edomu anali nao ana, woyamba Semaya, waciwiri Yozabadi, wacitatu Yowa, wacinai Sakara, wacisanu Netaneli,

5 wacisanu ndi cimodzi Amiyeli, wacisanu ndi ciwiri Isakara, wacisanu ndi citatu Peuletai; pakuti Mulungu adamdalitsa.

6 Kwa Semaya mwana wace yemwe kunabadwa ana, akulamulira nyumba ya atate wao; pakuti anali ngwazi zamphamvu.

7 Ana a Semaya: Otini, ndi Refaeli, ndi Obedi, Elzabadi, amene abale ao ndiwo odziwa mphamvu, Elihu, ndi Semakiya.

8 Onsewa ndiwo a ana a Obedi Edomu; iwo ndi ana ao, ndi abale ao, anthu odziwa mphamvu yakutumikira, makumi asanu ndi limodzi mphambu awiri a Obedi Edomu.

9 Ndi Meselemiya anali ndi ana, ndi abale odziwa mphamvu khumi mphambu asanu ndi atatu.

10 Hosa yemwe wa ana a Merari anali ndi ana, wamkuru ndi Simri; pakuti ngakhale sanali wobadwa woyamba, atate wace anamuyesa wamkuru;

11 waciwiri Hilikiya, wacitatu Tebaliya, wacinai Zekariya; ana ndi abale onse a Hosa ndiwo khumi ndi atatu.

12 Mwa iwowa munali magawidwe a odikira, mwa akulu a amuna akucita udikiro wao, monga abale ao, kutumikira m'nyumba ya Yehova.

13 Ndipo anacita maere ang'ono ndi akuru, monga mwa nyumba za makolo ao, kucitira zipata zonse.

14 Ndi maere a kum'mawa anagwera Selemiya. Ndipo anacitira maere Zekariya mwana wace, phungu wanzeru, ndi maere anamgwera kumpoto;

15 Obedi Edomu kumwela, ndi ana ace nyumba ya akatundu.

16 Supimu ndi Hosa kumadzulo, ku cipata ca Saleketi, ku mseu wokwerapo, udikiro pandunji pa udikiro.

17 Kum'mawa kunali Alevi asanu ndi mmodzi, kumpoto anai tsiku ndi tsiku, kumwela anai tsiku ndi tsiku, ndi a nyumba ya akatundu awiri ndi awiri.

18 Ku Parabara kumadzulo anai kumseu, ndi awiri ku Parabara.

19 Awa ndi magawidwe a odikira; a ana a Akora, ndi a ana a Merari.

20 Ndipo wa Alevi, Ahiya anayang'anira cuma ca nyumba ya Mulungu, ndi cuma ca zopatulika.

21 Ana a Ladani: ana a Ladani a Agerisoni, akuru a nyumba za makolo a Ladani Mgerisoni, Yehieli.

22 Ana a Yehieli: Zetamu ndi Yoeli mbale wace, oyang'anira cuma ca nyumba ya Yehova.

23 A Amirami, a Aizari, a Ahebroni, a Auziyeli;

24 ndi Sebueli mwana wa Gerisomu, mwana wa Mose, ndiye mkuru woyang'anira zuma.

25 Ndi abale ace a Eliezeri: Rehabiya mwana wace, ndi Yesava mwana wace ndi Yorramu mwana wace, ndi Zikiri mwana wace, ndi Selomoti mwana wace.

26 Selomoti amene ndi abale ace anayang'anira cuma conse ca zinthu zopatulika, zimene Davide mfumu ndi akuru a nyumba za akulu, akuru a zikwi ndi mazana, adazipatula.

27 Kutenga pa zofunkha kunkhondo, anapatulako kukonzera nyumba ya Yehova.

28 Ndipo zonse adazipatula Samueli mlauli, ndi Sauli mwana wa Kisi, ndi Abineri mwana wa Neri, ndi Yoabu mwana wa Zeruya; ali yense anapatula kanthu kali konse, anazisunga Selomoti ndi abale ace.

29 A Aizara: Kenaniya ndi ana ace anacita nchito ya pabwalo ya Israyeli, akapitao ndi oweruza mirandu.

30 A Ahebroni: Hasabiya ndi abale ace odziwa mphamvu cikwi cimodzi mphambu mazana asanu ndi awiri anayang'anira Israyeli tsidya lino la Yordano kumadzulo, kuyang'anira nchito yonse ya Yehova, ndi kutumikira mfumu.

31 Yeriya ndiye mkuru wa Ahebroni, wa Ahebroni monga mwa mibadwo ya nyumba za makolo. Caka ca makumi anai ca ufumu wa Davide anafunafuna, napeza mwa iwowa ngwazi zamphamvu ku Yazeri wa ku Gileadi.

32 Ndi abale ace ngwazi ndiwo zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi awiri, akuru a nyumba za makolo, amene mfumu Davide anaika akhale oyang'anira a Arubeni, ndi Agadi, ndi pfuko la Manase logawika pakati, pa zinthu zonse za Mulungu ndi zinthu za mfumu.

27

1 Ndipo ana a Israyeli monga mwa ciwerengo cao, kunena za akuru a nyumba za makolo ao, ndi akazembe a zikwi, ndi a mazana, ndi akapitao ao akutumikira mfumu mu nchito iri yonse ya magawidwe, akulowa ndi kuturuka mwezi ndi mwezi, miyezi yonse ya caka, cigawo ciri conse nca amuna zikwi makumi awiri mphambu zinai.

2 Woyang'anira cigawo coyamba ca mwezi, woyamba ndiye Yasobeamu mwana wa Zabidiyeli; m'cigawo mwace munali zikwi makumi awiri mphambu zinai.

3 Ndiye wa ana a Perezi, mkuru wa akazembe onse a khamu mwezi woyamba.

4 Woyang'anira cigawo ca mwezi waciwiri ndiye Dodai M-ahohi ndi cigawo cace; ndi Mikiloti mtsogoleri, ndi m'cigawo cace munali zikwi makumi awiri mphambu zinai.

5 Kazembe wacitatu wa khamu wa mwezi wacitatu ndiye Benaya mwana wa Yehoyada wansembe wamkuru; ndi m'cigawo mwacemunalinso zikwi makumi awiri mphambu zinai.

6 Benaya ameneyo ndiye wamphamvu uja wa makumi atatu aja, woyang'anira makumi atatu aja; woyang'anira cigawo cace ndi Amizabadi mwana wace.

7 Wacinai wa mwezi wacinai ndiye Asebeli mbale wa Yoabu, ndi pambuyo pace Zebadiya mwana wace; ndi m'cigawo mwace munali zikwi makumi awiri mphambu zinai.

8 Kazembe wacisanu wa mwezi wacisanu ndiye Samuti M-izra; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

9 Wacisanu ndi cimodzi wa mwezi wacisanu ndi cimodzi ndiye Ira mwana wa Ikesi Mtekoi; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

10 Wacisanu ndi ciwiri wa mwezi wacisanu ndi ciwiri ndiye Helezi Mpeloni wa ana a Efraimu; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

11 Wacisanu ndi citatu wa mwezi wacisanu ndi citatu ndiye Sibekai Mhusati wa Afera; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

12 Wacisanu ndi cinai wa mwezi wacisanu ndi cinai ndiye Abiezeri M-anatoti wa Abenjamini; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

13 Wakhumi wa mwezi wakhumi ndiye Maharai Mnetofati wa Azera; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

14 Wakhumi ndi cimodzi wa mwezi wakhumi ndi cimodzi ndiye Benaya Mpiratoni wa ana a Efraimu; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

15 Wakhumi ndi ciwiri wa mwezi wakhumi ndi ciwiri ndiye Heledai Mnetofati wa Otiniyeli; ndi m'cigawo mwace zikwi makumi awiri mphambu zinai.

16 Koma oyang'anira mafuko a lsrayeli ndi awa: wa Arubeni mtsogoleri wao ndiye Eliezeri mwana wa Zikiri; wa Asimeoni, Sefatiya mwana wa Maaka;

17 wa Alevi, Hasabiya mwana wa Kemueli; wa Aroni, Zadoki;

18 wa Yuda, Elihu mbale wina wa Davide; wa Isakara, Omri mwana wa Mikaeli;

19 wa Zebuluni, Isimaya mwana wa Obadiya; wa Nafitali, Yeremoti mwana wa Azrieli;

20 wa ana a Efraimu, Hoseya mwana wa Azaziya; wa pfuko la Manase logawika pakati, Yoeli mwana wa Pedaya;

21 wa pfuko la Manase logawika pakati m'Gileadi, Ido mwana wa Zekariya; wa Benjamini, Yasiyeli mwana wa Abineri;

22 wa Dani, Azareli mwana wa Yerohamu. Awa ndi akazembe a mapfuko a Israyeli.

23 Koma Davide sanawerenga iwo a zaka makumi awiri ndi ocepapo, pakuti Yehova adati kuti adzacurukitsa Israyeli ngati nyenyezi za kuthambo.

24 Yoabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga, koma sanatsiriza; ndi mkwiyo unagwera Israyeli cifukwa ca ici, ndipo ciwerengo cao sicinalembedwa m'buku la mbiri ya mfumu Davide.

25 Ndipo woyang'anira cuma ca mfumu ndiye Azimaveti mwana wa Adiyeli, ndi woyang'anira wa cuma ca m'minda, m'mizinda ndi m'miraga, ndi nyumba za nsanja, ndiye Yonatani mwana wa Uziya;

26 ndi woyang'anira iwo akugwira nchito ya m'munda yakulima nthaka ndiye Ezri mwana wa Kelubi;

27 ndi woyang'anira minda yamphesa ndiye Simeyi Mramati; ndi woyang'anira zipatso za minda yamphesa zisungike mosungiramo vinyo ndiye Zabidi Msifimi;

28 ndi woyang'anira mitengo yaazitona, ndi yamikuyu yokhala kuzidikha kunsi, ndiye Baala Hanani Mgederi; ndi woyang'anira zosungiramo mafuta ndiye Yoasi;

29 ndi woyang'anira ng'ombe zakudya m'Saroni ndiye Sitirai Msaroni; ndi woyang'anira ng'ombe za m'zigwa ndiye Safabi mwana wa Adilai;

30 ndi woyang'anira ngamira ndiye Obili M-israyeli; ndi woyang'anira aburu ndiye Yedeya Mmeronoti;

31 ndi woyang'anira zoweta zazing'ono ndiye Yazizi Mhagiri, Onsewa ndiwo akuru a zolemera zace za Davide.

32 Ndipo Yonatani atate wace wina wa Davide anali phungu, munthu wanzeru ndi mlembi; ndi Yehieli mwana wa Hakimoni anakhala ndi ana a mfumu;

33 ndi Ahitofeli anali phungu wa mfumu, ndi Husai M-ariki anali bwenzi la mfumu;

34 ndi wotsatana ndi Ahitofeli, Yehoyada mwana wa Benaya, ndi Abyatara; koma kazembe wa nkhondo ya mfumu ndiye Yoabu.

28

1 Pamenepo Davide anasonkhanitsa ku Yerusalemu akalonga Israyeli, a akalonga a mapfuko, ndi akuru a zigawo zakutumikira mfumu, ndi akulu a zikwi, ndi akuru a mazana, ndi akuru a zolemera zonse, ndi zoweta zonse za mfumu, ndi ana ace; pamodzi ndi akapitao ndi anthu amphamvu, ndiwo ngwazi zamphamvu onsewo.

2 Ndipo mfumu Davide anaima ciriri, nati, Mundimvere ine, abale anga ndi anthu anga, ine kumtima kwanga ndinafuna kulimangira likasa la cipangano la Yehova, ndi popondapo mapazi a Mulungu wathu nyumba yopumulira, ndipo ndidakonzeratu za nyumbayi.

3 Koma Mulungu anati kwa ine, Sudzamangira dzina langa nyumba, popeza ndiwe munthu wa nkhondo wokhetsa mwazi.

4 Komatu Yehova Mulungu wa Israyeli anasankha ine m'nyumba yonse ya atate wanga, ndikhale mfumu ya Israyeli kosatha; pakuti anasankhiratu Yuda akhale mtsogoleri, ndi m'nyumba ya Yuda nyumba ya atate wanga, ndi mwa ana a atate wanga ndinamkomera ndine, andilonge ufumu wa Israyeli yense;

5 ndi mwa ana anga onse (pakuti Yehova wandipatsa ana amuna ambiri), anasankha Solomo mwana wanga akhale pa mpando wacifumu wa ufumu wa Yehova kuweruza Israyeli.

6 Ndipo anati kwa ine, Solomo mwana wako ndiye adzandimangira nyumba yanga ndi mabwalo anga; pakuti ndamsankha akhale mwana wanga, ndipo Ine ndidzakhala atate wace.

7 Ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wace kosatha, akalimbika kucita malamulo anga ndi maweruzo anga monga lero lino.

8 Ndipo tsopano, pamaso pa Aisrayeli onse, khamu la Yehova, ndi m'makutu a Mulungu wathu, sungani, nimufunefune malamulo onse a Yehova Mulungu wanu, kuti mukhale nalo lanu lanu dziko lokoma ili, ndi kulisiyira ana anu pambuyo panu colowa cao kosalekeza.

9 Ndipo iwe Solomo mwana wanga, umdziwe Mulungu wa atate wako, umtumikire ndi mtima wangwiro ndi moyo waufulu; pakuti Yehova asanthula mitima yonse, nazindikira zolingirira zonse za maganizo; ukamfunafuna iye udzampeza, koma ukamsiya iye adzakusiya kosatha.

10 Cenjera tsono, pakuti Yehova anakusankha iwe umange nyumba ya malo opatulika; limbika, nucite.

11 Pamenepo Davide anapatsa Solomo mwana wace cifaniziro ca likole la kacisi, ndi ca nyumba zace, ndi ca zosungiramo cuma zace, ndi ca zipinda zosanjikizana zace, ndi ca zipinda zace za m'katimo, ndi ca kacisi wotetezerapo;

12 ndi cifaniziro ca zonse anali nazo mwa mzimu, ca mabwalo a nyumba ya Yehova, ndi ca zipinda zonse pozungulirapo, ca zosungiramo cuma za nyumba ya Mulungu, ndi ca zosungiramo cuma za zinthu zopatulika;

13 ndi ca magawidwe a ansembe ndi Alevi, ndi ca nchito zonse za utumiki wa nyumba ya Yehova, ndi ca zipangizo za utumiki wa nyumba ya Yehova;

14 ca golidi woyesedwa kulemera kwace wa zipangizo zagolidi, wa zipangizo zonse za nchito ya mtundu uli wonse; ca siliva wa zipangizo zasiliva woyesedwa kulemera kwace, wa zipangizo za nchito ya mitundu mitundu;

15 mwa kulemera kwacenso ca zoikapo nyali zagolidi, ndi nyali zace zagolidi, mwa kulemera kwace ca coikapo nyali ciri conse, ndi nyali zace; ndi ca zoikapo nyali zasiliva, siliva woyesedwa kulemera kwace wa coikapo nyali ciri conse, ndi nyali zace, monga mwa coikapo nyali ciri conse;

16 ndi golidi woyesedwa kulemera kwace wa magome a makate woonekera, wa gome liri lonse; ndi siliva wa magome asiliva,

17 ndi mitengo, ndi mbale zowazira, ndi zikho za golidi woona, ndi ca mitsuko yace yagolidi, woyesedwa kulemera kwace mtsuko uli wonse; ndi ca mitsuko yasiliva woyesedwa kulemera kwace mtsuko uli wonse;

18 ndi ca guwa la nsembe lofukizapo la golidi woyengetsa woyesedwa kulemera kwace, ndi cifaniziro ca gareta wa akerubi agolidi akufunyulula mapiko ao ndi kuphimba likasa la cipangano la Yehova.

19 Conseci, anati Davide, anandidziwitsa ndi kucilemba kucokera kwa dzanja la Yehova; ndizo nchito zonse za cifaniziro ici.

20 Ndipo Davide anati kwa Solomo mwana wace, Limbika, nulimbe mtima, nucicite; usaopa, kapena kutenga nkhawa; pakuti Yehova Mulungu, ndiye Mulungu wanga, ali nawe; sadzakusowa kapena kukutaya mpaka zitatha nchito zonse za utumiki wa nyumba ya Yehova.

21 Ndipo taona, pali zigawo za ansembe ndi Alevi, za utumiki wonse wa nyumba ya Mulungu; ndipo pamodzi nawe mu nchito iri yonse pali onse ofuna eni ace aluso, acite za utumiki uli wonse; akuru omwe ndi anthu onse adzacita monga umo udzanenamo.

29

1 Mfumu Davide ananenanso kwa khamu lonse, Mulungu wasankha mwana wanga Solomo yekha, ndiye mnyamata ndi wosakhwima; ndipo nchitoyi ndi yaikuru, pakuti cinyumbaci siciri ca munthu, koma ca Yehova Mulungu.

2 Ndi mphamvu yanga yonse tsono ndakonzeratu nyumba ya Mulungu wanga, golidi wa zija zagolidi ndi siliva wa zija zasiliva, ndi mkuwa wa zija zamkuwa, citsulo ca zija zacitsulo, ndi mtengo wa zija zamtengo, miyala yaberulo, ndi miyala yoikika, miyala yokometsera, ndi ya mawanga mawanga, ndi miyala ya mtengo wace ya mitundu mitundu ndi miyala yansangalabwe yocuruka.

3 Ndiponso popeza ndikondwera nayo nyumba ya Mulungu wanga, cuma cangacanga ca golidi ndi siliva ndiri naco ndicipereka ku nyumba ya Mulungu wanga, moenjezera ndi zonse ndazikonzeratu nyumba yopatulikayo;

4 ndico matalente zikwi zitatu za golidi, golidi wa Ofiri; ndi matalente zikwi zisanu ndi ziwiri a siliva woyengetsa, kumamatiza nazo makoma a nyumbazi;

5 golidi wa zija zagolidi, ndi siliva wa zija zasiliva, ndi za nchito ziri zonse akuzipanga manja a amisiri. Ndani uyo afuna mwini kudzipatulira kwa Yehova lero line?

6 Pamenepo akuru a nyumba za makolo, ndi akuru a mafuko a Israyeli, ndi akuru a zikwi ndi a mazana pamodzi ndi iwo oyang'anira nchito ya mfumu, anapereka mwaufulu,

7 napereka ku utumiki wa nyumba ya Mulungu golidi matalente zikwi zisanu, ndi madariki zikwi khumi; ndi siliva matalente zikwi khumi, ndi mkuwa matalente zikwi khumi mphambu zisanu ndi zitatu, ndi citsulo matalente zikwi zana limodzi.

8 Ndipo amene anali nayo miyala ya mtengo wace anaipereka ku cuma ca nyumba ya Yehova, mwa dzanja la Yehieli Mgerisoni.

9 Ndipo anthu anakondwera popeza anapereka mwaufulu; pakuti ndi mtima wangwiro anapereka mwaufulu kwa Yehova; mfumu Davide yemwe anakondwera ndi cimwemwe cacikuru.

10 Motero Davide analemekeza Yehova pamaso pa khamu lonse, nati Davide, Wolemekezedwa Inu, Yehova Mulungu wa Israyeli, Atate wathu ku nthawi zomka muyaya.

11 Ukulu, ndi mphamvu, ndi ulemerero, ndi kulakika, ndi cifumu ndi zanu, Yehova; pakuti zonse zam'mwamba ndi pa dziko lap ansi ndi zanu; ufumu ndi wanu, Yehova; ndipo mwakwezeka mutu wa pa zonse.

12 Zolemera ndi ulemu zifuma kwanu, ndipo mucita ufumu pa zonse, ndi m'dzanja mwanu muli mphamvu yaikuru; kukuza ndi kupatsa onse mphamvu kuli m'dzanja lanu.

13 Motero tsono, Mulungu wathu, tikuyamikani ndi kulemekeza dzina lanu lokoma.

14 Kama ndine yani, ndi anthu anga ndiwo ayani, kuti tidzakhoza kupereka mwaufulu motere? popeza zonsezi zifuma kwanu; takupatsani zofuma ku dzanja lanu.

15 Pakuti ife ndife alendo pamaso panu, ndi ogonera, monga makolo athu onse; masiku athu a padziko akunga mthunzi, ndipo palibe kukhalitsa.

16 Yehova Mulungu wathu, zounjikika izi zonse tazikonzeratu kukumangirani Inu nyumba ya dzina lanu loyera zifuma ku dzanja lanu, zonsezi ndi zanu.

17 Ndidziwanso, Mulungu wanga, kuti muyesa mtima, nimukondwera nako kuongoka. Kama ine, ndi mtima wanga woongoka ndapereka zonsezi mwaufulu; ndipo tsopano ndaona mokondwera anthu anu okhala pompano, napereka kwa Inu mwaufulu.

18 Yehova Mulungu wa Abrahamu, wa Isake, ndi wa Israyeli makolo athu, musungitse ici kosatha m'cilingaliro ca maganizo a mtima wa anthu anu, nimulunjikitse mitima yao kwanu,

19 nimupatse Solomo mwana wanga mtima wangwiro kusunga malamulo anu, mboni zanu, ndi malemba anu, ndi kucita izi zonse, ndi kumanga cinyumbaci cimene ndakonzeratu mirimo yace,

20 Ndipo Davide anati kwa khamu lonse, Mulemekeze tsono Yehova Mulungu wanu. Ndi khamu lonse linalemekeza Yehova Mulungu wa makolo ao, nawerama, nalambira Yehova, ndi mfumu.

21 Ndipo anamphera Yehova nsembe, napereka nsembe zopsereza kwa Yehova m'mawa mwace mwa tsiku lija, ndizo ng'ombe cikwi cimodzi, nkhosa zamphongo cikwi cimodzi, ndi ana a nkhosa cikwi cimodzi, pamodzi ndi nsembe zao zothira, ndi nsembe zocuruka za Aisrayeli onse:

22 nadya namwa pamaso pa Mulungu tsiku lomwelo ndi cimwemwe cacikuru. Ndipo analonga ufumu Solomo mwana wa Davide kaciwiri, namdzozera Yehova akhale kalonga, ndi Zadoki akhale wansembe.

23 Momwemo Solomo anakhala pa mpando wacifumu wa Yehova, ndiye mfumu m'malo mwa Davide atate wace, nalemerera, nammvera iye Aisrayeli onse.

24 Ndi akuru onse, ndi amuna amphamvu onse, ndi ana amuna onse omwe a mfumu Davide, anagonjeratu kwa Solomo mfumu.

25 Ndipo Yehova anakuza Solomo kwakukuru pamaso pa Aisrayeli onse, nampatsa ulemerero wacifumu, wakuti, asanakhale iyeyu, panalibe mfumu ya Israyeli inali nao wotero.

26 Momwemo Davide mwana wa Jese adakhala mfumu ya Aisrayeli onse.

27 Ndipo nthawi yoti anakhala mfumu ya Israyeli ndiyo zaka makumi anai; zaka zisanu ndi ziwiri anakhala mfumu m'Hebroni, ndi zaka makumi atatu anakhala mfumu m'Yerusalemu.

28 Nafa atakalamba bwino, wocuruka masiku, zolemera, ndi ulemerero; ndi Solomo mwana wace anakhala mfumu m'malo mwaceo

29 Zocita mfumu Davide tsono, zoyamba ndi zotsiriza, taonani, zalembedwa m'buku la mau a Samueli mlauli, ndi m'buku la mau a Natani mneneri, ndi m'buku la mau a Gadi mlauli;

30 pamodzi ndi za ufumu wace wonse, ndi mphamvu yace, ndi za nthawizo zidampitira iye, ndi Israyeli, ndimaufumu onse a maiko.