1 KATUNDU adamuona Habakuku
2 Yehova, ndidzapfuula mpaka liti osamva Inu? ndipfuulira kwa Inu za ciwawa, koma simupulumutsa.
3 Mundionetseranji zopanda pace, ndi kundionetsa zobvuta? pakuti kufunkha ndi ciwawa ziri pamaso panga; ndipo pali ndeli nauka makani.
4 Pakuti cilamulo calekeka, ndi ciweruzo siciturukira konse; popeza woipa azinga wolungama, cifukwa cace ciweruzo cituruka copindika.
5 Penyani mwa amitundu, penyetsetsani, nimudabwe kwakukuru, pakuti ndicita nchito masiku anu, imene simudzabvomera cinkana akufotokozerani.
6 Pakuti taonani, ndiukitsa Akasidi, mtundu uja wowawa ndi waliwiro, wopitira, pa citando ca dziko lapansi, kulowa m'malo mosati mwao, mukhale mwao mwao.
7 Ali oopsa, acititsa mantha, ciweruzo cao ndi ukulu wao zituruka kwa iwo eni.
8 Akavalo ao aposa anyalugwe liwiro lao, aposa mimbulu ya madzulo ukali wao, ndipo apakavalo ao atanda; inde apakavalo ao afumira kutali; auluka ngati ciombankhanga cofulumira kudya.
9 Adzera ciwawa onsewo; nkhope zao zikhazikika zolunjika m'tsogolo; asonkhanitsa andende ngati mcenga,
10 Inde anyoza mafumu, aseka akalonga; aseka linga liri lonse; popeza aunjika dothi, nalilanda.
11 Pamenepo adzapitirira ngati mphepo, oadzalakwa ndi kuparamula, iye amene aiyesa mphamvu yace mulungu wace.
12 Si ndinu wacikhalire, Yehova Mulungu wanga, wopatulika wanga? sitidzafa. Yehova munamuikiratu kuti aweruzidwe; ndipo Inu, Thanthwe, munamkhazika kuti alangidwe.
13 Inu wa maso osalakwa, osapenya coipa, osakhoza kupenyerera cobvuta, mupenyereranji iwo akucita mocenjerera, ndi kukhala cete pamene woipa ammeza munthu wolungama woposa iye mwini;
14 ndi kuyesa anthu ngati nsomba za m'nyanja, ngati zokwawa zopanda wakuzilamulira.
15 Aziwedza zonse ndi mbedza, azigwira m'ukonde wace, nazisonkhanitsa m'khoka mwace; cifukwa cace asekera nakondwerera.
16 Cifukwa cace aphera nsembe ukonde wace, nafukizira khoka lace, pakuti mwa izi gawo lace lilemera, ndi cakudya cace cicuruka.
17 Kodi m'mwemo adzakhuthula m'ukonde mwace osaleka kuphabe amitundu?
1 Ndidzaima pa dindiro langa ndi kudziika palinga, ndipo ndidzayang'anira ndione ngati adzanenanji mwa ine, ngatinso ndidzamyankha ciani pa coneneza canga.
2 Ndipo Yehova anandiyankha nati, Lembera masomphenyawo, nuwacenutse pamagome, kuti awawerenge mofulumira.
3 Pakuti masomphenyawo alindira nyengo yoikidwiratu, ndipo afulumirira potsirizira pace, osanama; akacedwa uwalindirire; popeza afika ndithu, osazengereza.
4 Taonani, moyo wace udzikuza, wosaongoka m'kati mwace; koma wolungama adzakhala ndi moyo mwa cikhulupiriro cace.
5 Ndiponso vinyo ngwonyenga, ngati munthu wodzikuza, wosakhala kwao; wakukulitsa cikhumbo cace ngati kunsi kwa manda, akunga imfa, yosakhuta, koma adzisonkhanitsira amitundu onse, nadzimemezera mitundu yonse ya anthu.
6 Kodi sadzamnenera fanizo onsewo, ndi mwambi womnyodola, ndi kuti, Tsoka iye wocurukitsa zimene siziri zace! mpaka liti? iye wodzisenzera zigwiriro.
7 Sadzauka kodi modzidzimuka iwo amene adzakuluma, ndi kugalamuka iwo amene adzakugwedezetsa; ndipo udzakhala zofunkha zao?
8 Popeza iwe wafunkha amitundu ambiri, otsala onse a mitundu ya anthu adzakufunkha iwe; cifukwa ca mwazi wa anthu, ndi ciwawa cocitikira dziko, mudzi, ndi onse okhalamo.
9 Tsoka iye wakupindulitsira nyumba yace phindu loipa, kuti aike cisanja cace ponyamuka, kuti alanditsidwe m'dzanja la coipa!
10 Wapangira nyumba yako camanyazi, pakuononga mitundu yambiri ya anthu, ndipo wacimwira moyo wako.
11 Pakuti mwala wa m'khoma upfuula, ndi mtanda wa kuphaso udzaubvomereza.
12 Tsoka tye wakumanga mudzindi mwazi, nakhazikitsa mudzi ndi cisalungamo!
13 Taonani, sicicokera kwa Yehova wa makamu kodi kuti mitundu ya anthu ingogwirira moto nchito, ndi anthu angodzilemetsa pa zopanda pace?
14 Pakuti dziko lapansi lidzadzazidwa ndi cidziwitso ca ulemerero wa Yehova, monga madzi aphimba pansi panyanja.
15 Tsoka wakuninkha mnzace cakumwa, ndi kuonjezako mankhwala ako, ndi kumledzeretsa, kuti upenyerere manyazi ao!
16 Udzazidwa nao manyazi m'malo mwa ulemerero; imwa iwenso, nukhale wosadulidwa; cikho ca dzanja lamanja la Yehova cidzatembenukira iwe, ndi kusanza kwa manyazi kudzakhala pa ulemerero wako,
17 Pakuti ciwawa cidacitikira Lebano cidzakukuta, ndi cionongeko ca nyama cidzakuopsa; cifukwa ca mwazi wa anthu, ndi ciwawa cocitidwira dziko, mudzi, ndi onseokhalamo.
18 Apindulanji nalo fano losema, kuti wakulipanga analisema; fano loyenga ndi mphunzitsi wamabodza, kuti wakulipanga alikhulupirira, ata panga matafano osanena mau?
19 Tsoka iye wakunena kwa mtengo, Galamuka; ndi kwa mwala wosalankhula, Nyamuka Kodi ici ciphunzitsa? Taona cakutidwa ndi golidi ndi siliva, ndi m'kati mwace mulibe mpweya konse.
20 Koma Yehova ali m'Kacisi wace wopatulika; dziko lonse lapansi ale, cete pamaso pace.
1 Pemphero la Habakuku mneneri, pa Sigionoto.
2 Yehova, ndinamva mbiri yanu ndi mantha; Yehova, tsitsimutsani nchito yanu pakati pa zaka, Pakati pa zaka mudziwitse; Pa mkwiyo mukumbukile cifundo.
3 Mulungu anafuma ku Temani, Ndi Woyerayo ku phiri la Parana. Ulemerero wace unaphimba miyamba, Ndi dziko lapansi linadzala ndi kumlemekeza.
4 Ndi kunyezimira kwace kunanga kuunika; Anali nayo mitsitsi ya dzuwa yoturuka m'dzanja lace. Ndi komweko kunabisika mphamvu yace.
5 Patsogolo pace panapita mliri, Ndi makara amoto anaturuka pa mapaziace.
6 Anaimirira, nandengulitsa dziko lapansi; Anapenya, nanjenjemeretsa amitundu; Ndi mapiri acikhalire anamwazika, Zitunda za kale lomwe zinawerama; Mayendedwe ace ndiwo a kale lomwe.
7 Ndinaona mahema a Kusani ali mkusauka; Nsaru zocinga za dziko la Midyani zinanjenjemera.
8 Kodi Yehova anaipidwa nayo mitsinje? Mkwiyo wanu unali pamitsinje kodi, Kapena ukali wanu panyanja, Kuti munayenda pa akavalo anu, Pa magareta anu a cipulumutso?
9 Munapombosola uta wanu; Malumbiro analumbirira mafuko anali mau oona. Munang'amba dziko lapansi ndi mitsinje.
10 Mapiri anakuonani, namva zawawa; Cigumula ca madzi cinapita; Madzi akuya anamveketsa mau ace, Nakweza manja ace m'mwamba.
11 Dzuwa ndi mwezi zinaima njera mokhala mwao; Pa kuunika kwa mibvi yanu popita iyo. Pa kung'anipa kwa nthungo yanu yonyezimira.
12 Munaponda dziko ndi kulunda, Munapuntha amitundu ndi mkwiyo.
13 Munaturukira cipulumutso ca anthu anu, Cipulumutso ca odzozedwa anu; Munakantha mutu wa nyumba yawoipa, Ndi kufukula maziko kufikira m'khosi.
14 Munapyoza ndi maluti ace mutu wa ankhondo ace; Anadza ngati kabvumvulu kundimwaza; Kukondwerera kwao kunanga kufuna kutha ozunzika mabisika.
15 Munaponda panyanja ndi akavaloanu, Madzi amphamvu anaunjikana mulu.
16 Ndinamva, ndi m'mimba mwanga munabwadamuka, Milomo yanga inanthunthumira pamau, M'mafupa mwanga mudalowa cibvundi, ndipo ndinanjenjemera m'malo mwanga; Kuti ndipumule tsiku lamsauko, Pamene akwerera anthu kuti ayambane nao ndi makamu.
17 Cinkana mkuyu suphuka, Kungakhale kulibe zipatso kumpesa; Yalephera nchito ya azitona, Ndi m'minda m'mosapatsa cakudya; Ndi zoweta zacotsedwa kukhola, Palibenso ng'ombe m'makola mwao;
18 Koma ndidzakondwera mwa Yehova, Ndidzasekerera mwa Mulungu wa cipulumutso canga.
19 Yehova, Ambuye, ndiye mphamvuyanga, Asanduliza mapazi anga ngati a mbawala, Nadzandipondetsa pa misanje yanga.