1

1 PAULO, ndi Silvano, ndi Timoteo, kwa Mpingo wa Atesalonika mwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Kristu: Cisomo kwa inu ndi mtendere.

2 Tiyamika Mulungu nthawi zonse cifukwa ca inu nonse, ndi kukumbukila inu m'mapemphero athu;

3 ndi kukumbukila kosalekeza nchito yanu ya cikhulupiriro, ndi cikondi cocitacita, ndi cipiriro ca ciyembekezo ca Ambuye wathu Yesu Kristu, pamaso pa Mulungu Atate wathu;

4 podziwa, abale okondedwa ndi Mulungu, cisankhidwe canu,

5 kuti Vthenga Wabwino wathu sunadza kwa inu m'mau mokha, komatunso mumphamvu, ndi mwa Mzimu Woyera, ndi m'kucuruka kwakukuru; monga mudziwa tinakhala onga otani mwa inu cifukwa ca inu.

6 Ndipo munayamba kukhala akutsanza athu, ndi a Ambuye, m'mene mudalandira mauwo m'cisautso cambiri, ndi cimwemwe ca Mzimu Woyera;

7 kotero kuti munayamba kukhala inu citsanzo kwa onse akukhulupira m'Makedoniya ndi m'Akaya.

8 Pakuti kuturuka kwa inu kudamveka mau a Ambuye, osati m'Makedoniya ndi Akaya mokha, komatu m'malo monse cikhulupiriro canu ca kwa Mulungu cidaturuka; kotero kuti sikufunika kwa ife kulankhula kanthu.

9 Pakuti iwo okha alalikira za ife, malowedwe athu a kwa inu anali otani; ndi kuti munatembeoukira kwa Mulungu posiyana nao mafano, kutumikira Mulungu weni weni wamoyo,

10 ndi kulindirira Mwana wace acokere Kumwamba, amene anamuukitsa kwa akufa, Yesu, wotipulumutsa ife ku mkwiyo ulinkudza.

2

1 Pakuti, abale, mudziwa nokha malowedwe athu a kwa inu, kuti sanakhala opanda pace;

2 koma tingakhale tidamva zowawa kale, ndipo anaticitira cipongwe, monga mudziwa, ku Filipi, tinalimbika pakamwa mwa Mulungu wathu kulankhula ndi inu Uthenga Wabwino wa Mulungu m'kutsutsana kwambiri.

3 Pakuti kudandaulira kwathu sikucokera kukusocera, kapena kucidetso, kapena m'dnyengo;

4 komatu monga Mulungu anatibvomereza kutiikiza Uthenga Wabwino, kotero tilankhula; osati monga okondweretsa anthu, koma Mulungu; amene ayesa mitima yathu.

5 Pakuti sitinayenda nao mau osyasyalika nthawi iri yonse, monga mudziwa, kapena kupsiniira msiriro, mboni ndi Mulungu;

6 kapena sitinakhala ofuna ulemerero wa kwa anthu, kapena kwa inu, kapena kwa ena, tingakhale tinali nayo mphamvu yakukulemetsanl monga atumwi a Kristu.

7 Komatu tinakhala ofat sa pakati pa inu, monga m'mene mlezi afukata ana ace a iye yekha;

8 kotero ife poliralira inu, tinabvomera mokondwera kupereka kwa inu si Uthenga Wabwino wa Mulungu wokha, komanso moyo wathu, popeza mudakhala okondedwa kwa ife.

9 Pakuti mukumbukila, abale, cigwiritso cathu ndi cibvuto cathu; pocita usiku ndi usana, kuti tingalemetse wina wa inu, tinalalikira kwa inu Uthenga Wabwino wa Mulungu.

10 Inu ndinu mboni, Mulungunso, kuti tinakhala oyera mtima ndi olungama ndi osalakwa kwa inu akukhulupirira;

11 monga mudziwa kuti tinacitira yense wa inu pa yekha, monga atate acitira ana ace a iye yekha, ndi kukudandaulirani, ndi kukusangalatsani ndi kucita umboni,

12 kuti muyende koyenera Mulungu, amene akuitanani inu mulowe ufumu wace wa iye yekha, ndi ulemerero.

13 Ndipo mwa icinso ife tiyamika Mulungu kosalekeza, kuti, pakulandira mau a Uthenga wa Mulungu, simunawalandira monga mau a anthu, komatu monga momwe ali ndithu, mau a Mulungu, amenenso acita mwa inuokhulupirira.

14 Pakuti inu, abale, munayamba kukhala akutsanza a Mipingo ya Mulungu yokhala m'Yudeya mwa Kristu Yesu; popeza zomwezi mudazimva kowawa nelinunso pamanja pa a mtundu wanu wa inu nokha, monganso iwowapa manja a Ayuda;

15 amene adaphanso Ambuye Yesu, ndi aneneri, natilondalonda ife, ndipo sakondweretsa Mulungu, natsutsana nao anthu onse;

16 natiletsa ife kuti tisalankhule ndi akunja kuti apulumutsidwe; kudzaza macimo ao nthawi zonse; koma mkwiyo wafika pa iwo kufikira cimariziro.

17 Koma ife, abale, angakhale adaticotsa kusiyana nanu kanthawi, osapenyana maso, koma kusiyana mtima ai, tinayesetsa koposa kuona nkhope yanu ndi cilakolako cacikuru;

18 cifukwa tinafuna kudza kwa inu, inedi Paulo ndatero kamodzi kapena kawiri; koma Satana anatiletsa.

19 Pakuti ciyembekezo cathu, kapena cimwemwe, kapena korona wakudzitamandira naye nciani? si ndinu nanga pamaso pa Ambuye wathu Yesu m'kufika kwace?

20 Pakuti inu ndinu ulemerero wathu ndi cimwemwe cathu.

3

1 Cifukwa cace, posakhoza kulekereranso, tidabvomereza mtima atisiye tokhaku Atene;

2 ndipo tinatuma Timoteo, mbale wathuyo ndi mtumiki wa Mulungu m'Uthenga Wabwino wa Kristu, kuti akhazikitse inu; ndi kutonthoza inu za cikhulupiriro canu;

3 kuti asasunthike wina ndi zisautso izi, pakuti mudziwa nokha kuti adatiika ife ticite izi.

4 Pakutinso, pamenetinali ndi inu tinakuuziranitu kuti tidzamva zisautso; monga kudacitika, monganso mudziwa.

5 Mwa ici inenso, posalekereranso, ndinatuma kukazindikira cikhulupiriro canu, kuti kaperta: woyesa akadakuyesani, ndipo cibvuto cathu cikadakhala copanda pace.

6 Koma tsopano pofika Timoteo kwathu kucokera kwa inu, ndi kutifotokozera mbiri yokoma ya cikhulupiriro ndi cikondano canu, ndi kuti mutikumbukila bwino masiku onse, pokhumba kutiona ife, monganso ire kukuonani inu;

7 cifukwa ca ici tasangalala pa inu, abale, m'kupsinjika kwathu konse ndi cisautso cathu conse, mwa cikhulupiriro canu;

8 pakuti tsopano tiri ndi moyo, ngati inu mucirimika mwa Ambuye.

9 Pakuti tikhoza kubwezera kwa Mulungu ciyamiko canji cifukwa ca inu, pa cimwemwe conse tikondwera naco mwa inu pamaso pa Mulungu wathu;

10 ndi kucurukitsa mapemphero athu usiku ndi usana kuti tikaone nkhope yanu, ndi kukwaniritsa zoperewera pa cikhulupiriro canu?

11 Koma Mulungu Atate wathu mwini yekha, ndi Ambuye wathu Yesu atitsogolere m'njira yakufika kwa inu;

12 koma Ambuye akukulitseni inu, nakueurukitseni m'cikondano wina kwa mnzace ndi kwa anthu onse, monganso ife titero kwa inu;

13 kuti akakhazikitse mitima yanu yopanda cifukwa m'ciyero pamaso pa Mulungu Atate wathu, pakufika Ambuye wathu Yesu pamodzi ndi oyera mtima ace onse.

4

1 Cotsalira tsono, abale, tikupemphani ndi kukudandaulirani mwa Ambuye Yesu, kuti, monga munalandira kwa ife mayendedwe okoma, muyenera kuyendanso ndi kukondweretsa Mulungu, monganso mumayenda, eurukani koposa momwemo.

2 Pakuti mudziwa malangizo amene tinakupatsani mwa Ambuye Yesu.

3 Pakuti ici ndi cifuniro ca Mulungu, ciyeretso canu, kuti mudzipatule kudama;

4 yense wa inu adziwe kukhala naco cotengera cace m'ciyeretso ndi ulemu,

5 kosati m'eiliro ca cilakolako conyansa, monganso amitundu osadziwa Mulungu;

6 asapitirireko munthu, nanyenge mbale wace m'menemo, cifukwa Ambuye ndiye wobwezera wa izi zonse, monganso tinakuuziranitu, ndipo tinacitapo umboni.

7 Pakuti Mulungu sanaitana ife titsate cidetso, koma ciyeretso.

8 Cifukwa cace iye wotaya ici, sataya munthu, komatu Mulungu, wakupatsa Mzimu wace Woyera kwa inu.

9 Koma kunena za cikondano ca pa abale sikufunika kuti akulembereni; pakuti wakukuphunzitsani ndi Mulungu, kuti mukondane wina ndi mnzace;

10 pakutinso munawacitira ici abale onse a m'Makedoniya lonse. Koma tikudandaulirani, abale, mueurukireko koposa,

11 ndi kuti muyesetse kukhala cete ndi kucita za inu eni ndi kugwira nchito ndi manja anu, monga tinakuuzani;

12 kuti mukayende oona mtima pa iwo a kunja, ndi kukhala osasowa kanthu.

13 Koma sitifuna, abale, kuti mukhale osadziwa za iwo akugona; kuti mungalire monganso otsalawo, amene alibe ciyembekezo.

14 Pakuti ngati tikhulupirira kuti Yesu adamwalira, nauka, koteronso Mulungu adzatenga pamodzi ndi iye iwo akugona mwa Yesu.

15 Pakuti ici tinena kwa inu m'mau a Ambuye, kuti ife okhala ndi moyo, otsalira kufikira kufikanso kwa Ambuye, sitidzatsogolera ogonawo.

16 Pakuti Ambuye adzatsika Kumwamba mwini yekha ndi mpfuu, ndi mau a mngelo wamkuru, ndi lipenga la Mulungu; ndipo akufa mwa Ambuye adzayamba kuuka;

17 pamenepo ife okhala ndi moyo, otsalafe, tidzakwatulidwa nao pamodzi m'mitambo, kukakomana ndi Ambuye mumlengalenga, ndipo potero tidzakhala ndi Ambuye nthawi zonse.

18 Comweco, tonthozanani ndi mau awa,

5

1 Koma za nthawizo ndi nyengozo, abale, sikufunika kuti tidzakulemberani,

2 Pakuti inu nokha mudziwa bwino kuti tsiku la Ambuye lidzadza monga mbala usiku,

3 Pamene angonena, Mtendere ndi mosatekeseka, pamenepo cionongeko cobukapo cidzawagwera, monga zowawa mkazi wa pakati; ndipo sadzapulumuka konse.

4 Kama inu, abale, simuli mumdima, kuti tsikulo likakugwereni monga mbala;

5 pakuti inu nonse muli ana a kuunika, ndi ana a usana; sitiri a usiku, kapena a mdima;

6 cifukwa cace tsono tisagone monga otsalawo, komatu tidikire, ndipo tisaledzere,

7 Pakuti iwo akugona agona usiku; ndi iwo akuledzera aledzera usiku.

8 Koma ife popeza tiri a usana tisaledzere, titabvala capacifuwa ca cikhulupiriro ndi cikondi; ndi cisoti ciri ciyembekezo ca cipulumutso.

9 Pakuti Mulungu sanatiika ife tilawe mkwiyo, komatu kuti tilandire cipulumutso mwa Ambuye wathu Yesu Kristu,

10 amene anafa m'malo mwathu, kuti, tingakhale tidikira, tingakhale tigona, tikakhale ndi moyo pamodzi ndi Iye.

11 Mwa ici cenjezanani, ndipo mangiriranani wina ndi mnzace, monganso mumacita,

12 Koma, abale, tikupemphani, dziwani iwo akugwiritsa nchito mwa inu, nakhala akulu anu mwa Ambuye, nakuyatnbirirani inu;

13 ndipo muwacitire ulemu woposatu mwa cikondi, cifukwa ca nchito yao. Khalani mumtendere mwa inu nokha.

14 Koma tidandaulira inu abale, yambirirani ampwayi, limbikitsani amantha mtima? cirikizani ofok a, mukhale oleza mtima pa onse.

15 Penyani kuti wina asabwezere coipa womcitira coipa; komatu nthawi zonse mutsatire cokoma, kwa anzanu, ndi kwa onse.

16 Kondwerani nthawi zonse;

17 Pempherani kosaleka;

18 M'zonse yamikani; pakuti ici ndi cifuniro ca Mulungu ca kwa inu, mwa Kristu Yesu.

19 Musazime Mzimuyo;

20 Musanyoze maaenero;

21 Yesani zonse; sungani cokomaco,

22 Mupewe maonekedwe onse a coipa.

23 Ndipo Mulungu wa mtendere yekha ayeretse inu konsekonse; ndipo mzimu wanu ndi moyo wanu ndi thupi lanu zisungidwe zamphumphu, zopanda cirema pa kudza kwace kwa: Ambuye wathu Yesu Kristu.

24 Wakuitana inu ali wokhulupirika, amenensoadzacicita.

25 Abale, z tipempherereni ife.

26 1 Lankhulani abale onse ndi cipsompsono copatulika.

27 Ndikulumbirirani pa Ambuye kuti 2 kalatayu awerengedwe kwa abale onse.

28 Cisomo ca Ambuye wathu Yesu Kristu cikhale nanu.