1

1 WODALA munthuyo wosayenda mu uphungu wa oipa, Kapena wosaimirira m'njira ya ocimwa, Kapena wosakhala pansi pa bwalo la onyoza.

2 Komatu m'cilamulo ca Yehova muli cikondwerero cace; Ndipo m'cilamulo cace amalingima usana ndi usiku.

3 Ndiye akunga mtengo wooka pa mitsinje ya madzi; Wakupatsa cipatso cace pa nyengo yace, Tsamba lace lomwe losafota; Ndipo zonse azicita apindula nazo.

4 Oipa satero ai; Koma akunga mungu wouluka ndi mphepo.

5 Cifukwa cace oipa sadzaimirira pa mlanduwo, Kapena ocimwa mu msonkhano wa olungama.

6 Pakuti Yehova adziwa mayendedwe a olungama; Koma mayendedwe a oipa adzatayika.

2

1 Aphokoseranji amitundu. Nalingiriranji anthu zopanda pace?

2 Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi, Nacita upo akulu pamodzi, Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wace, ndi kuti.

3 Tidule zomangira zao, Titaye nsinga zao.

4 Wokhala m'mwambayo adzaseka; Ambuye adzawanyoza.

5 Pomwepo adzalankhula nao mu mkwiyo wace, Nadzawaopsa m'ukali wace:

6 Koma Ine ndadzoza mfumu yanga Pa Ziyoni, phiri langa loyera.

7 Ndidzauza za citsimikizo: Yehova ananena ndi Ine, Iwe ndiwe Mwana wanga; Ine lero ndakubala.

8 Undifunse, ndipo ndidzakupatsa amitundu akhale colowa cako, Ndi malekezero a dziko lapansi akhale ako ako.

9 Udzawatyola ndi ndodo yacitsulo; Udzawaphwanya monga mbiya yawoumba.

10 Tsono, mafumu inu, citani mwanzeru: Langikani, oweruza inu a dziko lapansi.

11 Tumikirani Yehova ndi mantha, Ndipo kondwerani ndi cinthenthe.

12 Mpsompsoneni Mwanayo, kuti angakwiye, ndipo mungatayike m'njira, Ukayaka pang'ono pokha mkwiyo wace. Odala onse akumkhulupirira Iye.

3

1 Yehova! Ha! acuruka nanga akundisautsa ine! Akundiukira ine ndi ambiri.

2 Ambiri amati kwa moyo wanga, Alibe cipulumutso mwa Mulungu.

3 Ndipo Inu Yehova, ndinu cikopa canga; Ulemerero wanga, ndi wondiweramutsa mutu wanga.

4 Ndipfuula kwa Yehova ndi mau anga, Ndipo andiyankha m'phiri lace loyera,

5 Ndinagona ine pansi, ndinagona tulo; Ndinauka; pakuti Yehova anandicirikiza.

6 Sindidzaopa unyinji wa anthu akundizinga ine.

7 Ukani Yehova; ndipulumutseni, Mulungu wanga! Pakuti mwapanda adani anga onse patsaya; Mwawatyola mano oipawo.

8 Cipulumutso nca Yehova; Dalitso lanu likhale pa anthu anu.

4

1 Pakupfuula ine mundiyankhe, Mulungu wa cilungamo canga; Pondicepera mwandikulitsira malo: Ndicitireni cifundo, imvani pemphero langa.

2 Amuna inu, ulemu wanga udzakhala wamanyazi kufikira liti? Mudzakonda zacabe, ndi kufunafuna bodza kufikira liti?

3 Koma dziwani kuti Yehova anadzipatulira yekha womkondayo Adzamva Yehova m'mene ndimpfuulira Iye,

4 Citani cinthenthe, ndipo musacimwe: Nenani mumtima mwanu pakama panu, ndipo mukhale cete.

5 Iphani nsembe za cilungamo, Ndipo mumkhulupirire Yehova.

6 Ambiri amati, Adzationetsa cabwino ndani? Weramutsirani ife kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.

7 Mwapatsa cimwemwe mumtima mwanga, Cakuposa cao m'nyengo yakucuruka dzinthu zao ndi vinyo wao.

8 Ndi mtendere ndidzagona pansi, pomwepo ndidzagona tulo; Cifukwa Inu, Yehova, mundikhalitsa ine, ndikhale bwino.

5

1 Mverani mau anga, Yehova, Zindikirani kulingirira kwanga.

2 Tamvetsani mau a kupfuula kwanga, Mfumu yanga, ndi Mulungu wanga: Pakuti kwa Inu ndimapemphera,

3 M'mawa, Yehova, mudzamva mau anga; M'mawa, ndidzakukonzerani pemphero langa, ndipo ndidzadikira.

4 Pakuti Inu sindinu Mulungu wakukondwera naco coipa Mphulupulu siikhala ndi Inu.

5 Opusa sadzakhazikika pamaso panu: Mudana nao onse akucita zopanda pace.

6 Mudzaononga iwo akunena bodza: Munthu wokhetsa mwazi ndi wacinyengo, Yehova anyansidwa naye.

7 Koma ine, mwa kucuruka kwa cifundo canu ndidzalowa m'nyumba yanu: Ndidzagwada kuyang'ana Kacisi wanu woyera ndi kuopa Inu.

8 Yehova, munditsogolere m'cilungamo canu, cifukwa ca akundizondawo; Mulungamitse njira yanu pamaso panga.

9 Pakuti m'kamwa mwao mulibe mau okhazikika; M'kati mwao m'mosakaza; M'mero mwao ndi manda apululu: Lilime lao asyasyalika nalo.

10 Muwayese otsutsika Mulungu; Agwe nao uphungu wao: M'kucuruka kwa zolakwa zao muwapitikitse; Pakuti anapikisana ndi Inu.

11 Koma akondwere onse amene athawira kwa Inu, Apfuule mokondwera kosaleka, popeza muwafungatira; Nasekere mwa Inu iwo akukonda dzina lanu.

12 Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungamayo; Mudzamcinjiriza naco cibvomerezo ngati cikopa.

6

1 Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, Ndipo musandilange m'ukali wanu.

2 Mundicitire cifundo, Yehova; pakuti ndalefuka ine: Mundicize, Yehova; pakuti anthunthumira mafupa anga.

3 Moyo wanganso wanthunthumira kwakukuru; Ndipo Inu, Yehova, kufikira liti?

4 Bwererani Yehova, landitsani moyo wanga; Ndipulumutseni cifukwa ca kukoma mtima kwanu.

5 Pakuti muimfa m'mosakumbukila Inu: M'mandamo adzakuyamikani dani?

6 Ndalema nako kuusa moyo kwanga; Ndiyandamitsa kama wanga usiku wonse; Mphasa yanga ndiolobza ndi misozi yanga.

7 Lapuwala diso langa cifukwa ca cisoni; Lakalamba cifukwa ca onse akundisautsa.

8 Cokani kwa ine, nonsenu akucita zopanda pace; Pakuti wamva Yehova mau a kulira kwanaa,

9 Wamva Yehova kupemba kwanga; Yehova adzalandira pemphero langa.

10 Adzacita manyazi, nadzanthunthumira kwakukuru adani anga onse; Adzabwerera, nadzacita manyazi modzidzimuka,

7

1 Yehova Mulungu wanga, ndakhulupirira Inu: Mundipulumutse kwa onse akundilonda, nimundilanditse;

2 Kuti angamwetule moyo wanga ngati mkango, Ndi kuukadzula, wopanda wina wondilanditsa.

3 Yehova Mulungu wanga, ngati ndacita ici; Ngati m'manja anga muli cosalungama;

4 Ngati ndambwezera coipa iye woyanjana ndine; (Inde, ndamlanditsa wondisautsa kopanda cifukwa);

5 Mdani alondole moyo wanga, naupeze; Naupondereze pansi moyo wanga, Naukhalitse ulemu wanga m'pfumbi.

6 Ukani Yehova mu mkwiyo wanu, Nyamukani cifukwa ca ukali wa akundisautsa: Ndipo mugalamukire ine; mwalamulira ciweruzo.

7 Ndipo ukuzingeni msonkhano wa anthu; Ndipo pamwamba pao mubwerere kumka kumwamba.

8 Yehova aweruza anthu mlandu: Mundiweruze, Yehova, monga mwa cilungamo canga, ndi ungwiro wanga uli mwa ine.

9 Ithe mphulupulu ya anthu oipa, ndikupemphani, koma wolungamayo mumkhazikitse: Pakuti woyesa mitima ndi imso ndiye Mulungu wolungama.

10 Cikopa canga ciri ndi Mulungu, Wopulumutsa oongoka mtima.

11 Mulungu ndiye Woweruza walungama, Ndiye Mulungu wakukwiya masiku onse.

12 Akapanda kutembenuka munthu, Iye adzanola lupanga lace; Wakoka uta wace, naupiringidza.

13 Ndipo anamkonzera zida za imfa; Mibvi yace aipanga ikhale yansakali,

14 Taonani, ali m'cikuta ca zopanda pace; Anaima ndi cobvuta, nabala bodza.

15 Anacita dzenje, nalikumba, Nagwa m'mbuna yomwe anaikumba.

16 Cobvuta cace cidzambwerera mwini, Ndi ciwawa cace cidzamgwera pakati pamutu pace.

17 Ndidzayamika Yehova monga mwa cilungamo cace; Ndipo ndidzayimbira Yehova Wam'mwambamwamba.

8

1 Yehova, Ambuye wathu, Dzina lanu liposadi nanga pa dziko lonse lapansi! Inu amene munaika ulemerero wanu pa thambo la kumwamba.

2 M'kamwa mwa makanda ndi oyamwamunakhazikitsamphamvu, Cifukwa ca otsutsana ndi Inu, Kuti muwaletse mdani ndi wobwezera cilango.

3 Pakuona ine thambo la kumwamba lanu, nchito ya zala zanu, Mwezi ndi nyenyezi, zimene munazikhazika,

4 Munthu ndani kuti mumkumbukila? Ndi mwana wa munthu kuti muceza naye?

5 Pakuti munamcepsa pang'ono ndi Mulungu, Munambveka iye korona wa ulemerero ndi ulemu.

6 Munamcititsa ufumu pa nchito za manja anu; Mudagonjetsa zonse pansi pa mapazi ace;

7 Nkhosa ndi ng'ombe, zonsezo, Ndi nyama za kuthengo zomwe;

8 Mbalame za m'mlengalenga, ndi nsomba za m'nyanja. Zopita m'njira za m'nyanja.

9 Yehova, Ambuye wathu, Dzina lanu liposadi nanga pa dziko lonse lapansi!

9

1 Ndidzayamika Yehova ndi mtima wanga wonse; Ndidzawerengera zodabwiza zanu zonse.

2 Ndidzakondwerera ndi kusekera mwa Inu; Ndidzayimbira dzina lanu, Wam'mwambamwamba Inu.

3 Pobwerera m'mbuyo adani anga, Akhumudwa naonongeka pankhope panu,

4 Pakuti mwandiweruzira mlandu wanga; Mwakhala pa mpando wacifumu, Woweruza wolungama.

5 Mwadzudzula amitundu, mwaononga woipayo, Mwafafaniza dzina lao ku nthawi Yomka muyaya.

6 Adaniwo atha psiti, apululuka nthawi zonse; Ndipo midziyo mwaipasula, Cikumbukilo cao pamodzi catha.

7 Koma Yehova akhala cikhalire: Anakonzeratu mpando wacifumu wace kuti aweruze.

8 Ndipo Iyeyu adzaweruza dziko lapansi m'cilungamo, Nadzaweruza anthu molunjika.

9 Ndipo Yehova adzakhala msanje kwa iye wokhalira mphanthi. Msanje m'nyengo za nsautso;

10 Ndipo iwo akudziwa dzina lanu adzakhulupirira Inu; Pakuti, Inu Yehova, simunawasiya iwo akufuna Inu.

11 Yimbirani zoyamika Yehova, wokhala ku Ziyoni; Lalikirani mwa anthu nchito zace.

12 Pakuti Iye wofuna camwazi awakumbukila; Saiwala kulira kwa ozunzika.

13 Ndicitireni cifundo, Yehova; Penyani kuzunzika kwanga kumene andicitira ondidawo, Inu wondinyamula kundicotsa ku zipata za imfa;

14 Kuti ndibukitse lemekezo lanu lonse; Pa bwalo la mwana wamkazi wa Ziyoni, Ndidzakondwera naco cipulumutso canu.

15 Amitundu anagwa m'mbuna imene anaikumba: Lakodwa phazi lao muukonde anaucha.

16 Anadziwika Yehova, anacita kuweruza: Woipayo anakodwa ndi nchito ya manja ace.

17 Oipawo adzabwerera kumanda, Inde amitundu onse akuiwala Mulungu.

18 Pakuti sadzaiwalika nthawi zonse waumphawi, Kapena ciyembekezo ca ozunzika sicidzaonongeka kosatha.

19 Ukani, Yehova, asalimbike munthu; Amitundu aweruzidwe pankhope panu.

20 Muwacititse mantha, Yehova; Adziwe amitundu kuti ali anthu.

10

1 Muimiranji patari, Yehova? Mubisaliranji m'nyengo za nsautso?

2 Podzikuza woipa apsereza waumphawi; Agwe m'ciwembu anapanganaco.

3 Pakuti woipa adzitamira cifuniro ca moyo wace, Adalitsa wosirira, koma anyoza Yehova.

4 Woipa, monga mwa kudzikuza kwa nkhope yace, akuti, Sadzafunsira. Malingaliro ace onse akuti, Palibe Mulungu.

5 Mayendedwe ace alimbika nthawi zonse; Maweruzo anu ali pamwamba posaona iye; Adani ace onse awanyodola.

6 Ati mumtima mwace, Sindidzagwedezeka ine; Ku mibadwo mibadwo osagwa m'tsoka ine.

7 M'kamwa mwace mwadzala kutemberera ndi manyengo ndi kucenjerera; Pansi pa lilime lace pali cibvutitso copanda pace.

8 Akhala m'molalira midzi; Mobisalamo akupha munthu wosacimwa: Ambisira waumphawi nkhope yace,

9 Alalira monga mkango m'ngaka mwace; Alalira kugwira wozunzika: Agwira wozunzika, pakumkola m'ukonde mwace.

10 Aunthama, nawerama, Ndipo aumphawi agwa m'zala zace.

11 Anena m'mtima mwace, Mulungu waiwala; Wabisa nkhope yace; sapenya nthawi zonse,

12 Ukani, Yehova; samulani dzanja lanu, Mulungu; Musaiwale ozunzika.

13 Woipa anyozeranii Mulungu, Anena m'mtima mwace, Simudzafunsira?

14 Mwapenya; pakuti mumayang'anira cibvutitso ndi cisoni kuti acipereke m'manja mwanu; Waumphawi adzipereka kwa Inu; Wamasiye mumakhala mthandizi wace.

15 Thyolani mkono wa woipa; Ndipo wocimwa, mutsate coipa cace kufikira simucipezanso cina.

16 Yehova ndiye Mfumu ku nthawi yamuyaya; Aonongeka amitundu m'dziko lace.

17 Yehova, mwamva cikhumbo ca ozunzika: Mudzakhazikitsa mtima wao, mudzachereza khutu lanu:

18 Kuti muweruze mlandu wa amasiye ndi wokhalira mphanthi, Kuti munthu wa pa dziko lapansi angaonjeze kuopsa.

11

1 Ndakhulupirira Yehova: Mutani nkunena kwa moyo wanga, Thawirani ku phiri lanu ngati mbalame?

2 Pakuti, onani, oipa akoka uta, Apiringidza mubvi wao pansinga, Kuwaponyera mumdima oongoka mtima.

3 Akapasuka maziko, Wolungama angacitenji?

4 Yehova ali m'Kacisi wace woyera, Yehova, mpando wacifumu wace uli m'Mwamba; Apenyerera ndi maso ace, ayesa ana a anthu ndi zikope zace.

5 Yehova ayesa wolungama mtima: Koma moyo wace umuda woipa ndi iye wakukonda ciwawa.

6 Adzagwetsa pwata pwata misampha pa oipa; Moto ndi miyala yasuifure, ndi mphepo yoopsa zidzawagawikira m'cikho cao.

7 Pakuti Yehova ndiye wolungama; akonda zolungama: Woongoka mtima adzapenya nkhope yace.

12

1 Pulumutsani, Yehova; pakuti wofatsa wasowa; Pakuti okhulupirika acepa mwa ana a anthu.

2 Amanena za bodza munthu yense ndi mnansi wace: Amanena ndi mlomo wotyasika, ndi mitima iwiri.

3 Yehova adzadula milomo yonse yotyasika, Lilime lakudzitamandira:

4 Amene amati, Ndi lilime lathu tidzaposa; Milomo yathu nja ife eni; mbuye wa pa ife ndani?

5 Cifukwa ca kupasuka kwa ozunzika, cifukwa ca kuusa moyo kwa aumphawi, Ndiuka tsopano, ati Yehova; Ndidzamlonga mosungika muja alaka-lakamo.

6 Mau a Yehova ndi mau oona; Ngati siliva woyenga m'ng'anjo yadothi, Yoiyeretsa kasanu ndi kawiri.

7 Mudzawasunga, Yehova, Mudzawacinjirizira mbadwo uno ku nthawi zonse.

8 Oipa amayenda mozungulira-zungulira, Potamanda iwo conyansa mwa ana a anthu.

13

1 Mudzandiiwala ciiwalire, Yehova, kufikira liti? Mudzandibisira ine nkhope yanu kufikira liti?

2 Ndidzacita uphungu m'moyo mwanga kufikira liti, Pokhala ndi cisoni m'mtima mwanga tsiku lonse? Adzandiukira ine mdani wanga kufikira liti?

3 Penyani, ndiyankheni, Yehova Mulungu wanga: Penyetsani maso anga, kuti ndingagone tulo ta imfa;

4 Kuti anganene mdani wanga, Ndamlaka; Ndipo angakondwere otsutsana nane posunthika ine.

5 Koma ine ndakhulupira pa cifundo canu; Mtima wanga udzakondwera naco cipulumutso canu:

6 Ndidzayimbira Yehova, Pakuti anandicitira zokoma.

14

1 Waucitsiru amati mumtima mwace, Kulibe Mulungu. Acita zobvunda, acita nchito zonyansa; Kulibe wakucita bwino.

2 Yehova m'Mwamba anaweramira pa ana a anthu, Kuti aone ngati aliko wanzeru, Wakufuna Mulungu.

3 Anapatuka onse; pamodzi anabvunda mtima; Palibe wakucita bwino ndi mmodzi yense.

4 Kodi onse ocita zopanda pace sadziwa kanthu? Pakudya anthu anga monga akudya mkate, Ndipo saitana pa Yehova.

5 Pamenepa anaopa-opatu: Pakuti Mulungu ali mu mbadwo wa wolungama.

6 Munyazitsa uphungu wa wozunzika, Koma Yehova ndiye pothawira pace.

7 Mwenzi cipulumutso ca Israyeli citacokera ku Ziyoni! Pakubweretsa Yehova anthu ace a m'nsinga, Pamenepo adzakondwera Yakobo, nadzasekera Israyeli.

15

1 Yehova, ndani adzagonera m'cihema mwanu? Adzagonera ndani m'phiri lanu lopatulika?

2 Iye wakuyendayo mokwanira, nacita cilungamo, Nanena zoonadi mumtima mwace.

3 Amene sasinjirira ndi lilime lace, Sacitira mnzace coipa, Ndipo satola msece pa mnansi wace.

4 M'maso mwace munthu woonongeka anyozeka; Koma awacitira ulemu akuopa Yehova. Atalumbira kwa tsoka lace, sasintha ai.

5 Ndarama zace sakongoletsa mofuna phindu lalikuru, Ndipo salandira cokometsera mlandu kutsutsa wosacimwa. Munthu wakucita izi sadzagwedezeka ku nthawi zonse,

16

1 Ndisungeni ine, Mulungu: pakuti ndakhulupirira Inu.

2 Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Ambuye wanga: Ndiribe cabwino cina coposa Inu.

3 Za oyera mtima okhala pa dziko lapansi, Iwo ndiwo omveka mbiri, mwa iwowo muli cikondwero canga conse.

4 Zidzacuruka zisoni zao za iwo otsata mulungu wina: Sindidzathira nsembe zao zamwazi, Ndipo sindidzachula maina ao pakamwa panga,

5 Yehova ndiye gawo la colowa canga ndi cikho canga: Ndinu wondigwirira colandira canga,

6 Zingwe zandigwera mondikondweretsa; Inde cosiyira cokoma ndiri naco.

7 Ndidzadalitsa Yehova, amene anandicitira uphungu: Usikunso imso zanga zindilangiza.

8 Ndaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse: Popeza ali pa dzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.

9 Cifukwa cace wasekera mtima wanga, nukondwera ulemu wanga; Mnofu wanganso udzakhala mokhazikika.

10 Pakuti simudzasiya moyo wanga kumanda; Simudzalola wokondedwa wanu abvunde.

11 Mudzandidziwitsa njira ya moyo: Pankhope panu pali cimwemwe cokwanira; M'dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.

17

1 Yehova, imvani cilungamo, mverani mpfuu wanga; Cherani khutu ku pemphero langa losaturuka m'milomo ya cinyengo,

2 Pankhope panu paturuke ciweruzo canga; Maso anu apenyerere zolunjika,

3 Mwayesera mtima wanga; mwandizonda usiku; Mwandisuntha, simupeza kanthu; Ndatsimikiza mtima kuti m'kamwa mwanga simudzalakwa.

4 Za macitidwe a anthu, ndaceniera ndi mau a milomo yanu Ndingalowe njira za woononga.

5 M'mayendedwe anga ndasunga mabande anu, Mapazi anga sanaterereka.

6 Ine ndinakuitanani, pakuti mudzandiyankha, Mulungu: Cherani khutu lanu kwa ine, imvani mau anga.

7 Onetsani cifundo canu codabwiza, Inu wakupulumutsa okhulupirira Inu Kwa iwo akuwaukira ndi dzanja lanu lamanja.

8 Ndisungeni monga kamwana ka m'diso, Ndifungatireni mu mthunzi wa mapiko anu,

9 Kundilanditsa kwa oipa amene andipasula, Adani a pa moyo wanga amene andizinga.

10 Mafuta ao awatsekereza; M'kamwa mwao alankhula modzikuza.

11 Tsopano anatizinga m'mayendedwe athu: Apenyetsetsa m'maso kuti atigwetse pansi.

12 Afanana ndi mkango wofuna kumwetula, Ndi msona wa mkango wakukhala mobisalamo.

13 Ukani Yehova, Mumtsekereze, mumgwetse: Landitsani moyo wanga kwa woipa ndi lupanga lanu;

14 Kwa anthu, ndi dzanja lanu, Yehova, Kwa anthu a dziko lapansi pano amene colowa cao ciri m'moyo uno, Ndipo mimba yao muidzaza ndi cuma canu cobisika: Akhuta mtima ndi ana, Nasiyira ana amakanda zocuruka zao.

15 Koma ine ndidzapenyerera nkhope yanu m'cilungamo: Ndidzakhuta mtima ndi maonekedwe anu, pamene ndidzauka.

18

1 Ndikukondani, Yehova, mphamvu yanga.

2 Yehova ndiye thanthwe langa, ndi linga langa, ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga, ngaka yanga, ndidzakhulupirira Iye; Cikopa canga, nyanga ya cipulumutso canga, msanje wanga.

3 Ndidzaitanira Yehova, woyenera kutamandika: Ndipo adzandipulumutsa ine kwa adani anga.

4 Zingwe za imfa zinandizinga, Ndipo mitsinje ya zopanda pace inandiopsa.

5 Zingwe za manda zinandizinga: Misampha ya imfa inandifikira ine.

6 M'kusauka kwanga ndinaitana Yehova, Ndipo ndinakuwira Mulungu wanga; Mau anga anawamva m'Kacisi mwace, Ndipo mkuwo wanga wa pankhope pace unalowa m'makutu mwace.

7 Pamenepo linagwedezeka, ndi kutenthemera dziko lapansi. Ndi maziko a mapiri ananjenjemera Nagwedezeka, pakuti anakwiya iyeyo.

8 Unakwera utsi woturuka m'mphuno mwace: Ndi moto wa m'kamwa mwace unanyeka: Nuyakitsa makara.

9 Ndipo Iye anaweramitsa thambo, natsika; Ndipo pansi pa mapazi ace panali mdima bii.

10 Ndipo anaberekeka pa kerubi, nauluka; Nauluka msanga pa mapiko a mphepo,

11 Anaika mdima pobisala pace, hema wace womzinga; Mdima wa madzi, makongwa a kuthambo.

12 Mwa kucezemira kunali pamaso pace makongwa anakanganuka, Matalala ndi makala amoto.

13 Ndipo anagunda m'mwamba Yehova, Ndipo Wam'mwambamwamba anamvetsa liu lace; Matalala ndi makala amoto,

14 Ndipo anatuma mibvi yace nawabalalitsa; Inde mphezi zaunyinji, nawamwaza.

15 Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi, Nafukuka maziko a dziko lapansi, Mwa kudzudzula kwanu, Yehova, Mwa mpumo wa mpweya wa m'mphuno mwanu.

16 Anatuma kucokera m'mwamba, ananditenga; Anandibvuula m'madzi ambiri.

17 Anandipulumutsa ine kwa mdani wanga wamphamvu, Ndi kwa iwo ondida ine, pakuti anandiposa mphamvu.

18 Anandipeza ine tsiku la tsoka langa; Koma Yehova anali mcirikizo wanga.

19 Ananditurutsanso andifikitse motakasuka; Anandilanditsa, pakuti anakondwera ndi ine.

20 Yehova anandibwezera monga mwa cilungamo canga; Anandisudzula monga mwa kusisira kwa manja anga.

21 Pakuti ndasunga njira za Yehova, Ndipo sindinacitira coipa kusiyana ndi Mulungu wanga.

22 Pakuti maweruzo ace onse anali pamaso panga, Ndipo malemba ace sindinawacotsa kwa ine.

23 Ndipo ndinakhala wangwiro ndi iye, Ndipo ndinadzisunga wosacita coipa canga.

24 Ndimo anandisudzulira Yehova monga mwa cilungamo canga, Monga mwa kusisira kwa manja anga pamaso pace.

25 Pa wacifundo mukhala wacifundo Pa mumthu wangwiro mukhala wangwiro;

26 Pa woyera mtima mukhala woyera mtima; Pa wotsutsatsutsa mukhala wotsutsana naye.

27 Pakuti Inu muwapulumutsa anthu aumphawi; Koma maso okweza muwatsitsa.

28 Pakuti Inu muyatsa nyali yanga; Yehova, Mulungu wanga, aunikira mdima wanga.

29 Pakuti mwa Inu ndipyola khamu la anthu; Ndipo mwa Mulungu wanga ndilumphira linga.

30 Mulungu ndiyewangwiro m'njira zace; Mau a Yehova ngoyengeka; Ndiye cikopa ca onse okhulupirira Iye.

31 Pakuti Mulungu ndani wosati Yehova? Ndipo thanthwe ndani wosati Mulungu wathu?

32 Mulungu ndiye wondizingiza mphamvu m'cuuno, Nakonza njira yanga ikhale yangwiro.

33 Alinganiza mapazi anga ngati a nswala: Nandiimitsa pamsanje panga.

34 Aphunzitsa manja anga agwire nkhondo; Kuti walifuka uta wamkuwa ndi manja anga.

35 Ndipo mwandipatsa cikopa ca cipulumutso canu: Ndipo dzanja lamanja lanu landigwiriziza, Ndipo cifatso canu candikuza ine.

36 Mwandipondetsa patali patali, Sanaterereka mapazi anga.

37 Ndidzalondola adani anga, ndi kuwapeza: Ndipo sindidzabwerera asanathe psiti.

38 Ndidzawapyoza kuti sangakhoze kuuka: Adzagwa pansi pa mapazi anga,

39 Pakuti mwaudizingiza mphamvu m'cuuno ku nkhondoyo: Mwandigonjetsera amene andiukira.

40 Ndipo adani anga mwawalozetsa m'mbuyo kwa ine, Kuti ndipasule ondidawo.

41 Anapfuula, koma panalibewopulumutsa; Ngakhale kwa Yehova, koma sanawabvomereza.

42 Pamenepo ndinawapera ngati pfumbi la kumphepo; Ndinawakhuthula ngati matope a pabwalo.

43 Mwandipulumutsa pa zolimbana nane za anthu; Mwandiika mutu wa amitundu; Mtundu wa anthu sindinaudziwa udzanditumikira.

44 Pakumva m'khutu za ine adzandimvera: Alendo adzandigonjera monyenga.

45 Alendo adzafota, Nadzaturuka monjenjemera m'ngaka mwao.

46 Yehova ngwa moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa; Nakwezeke Mulungu wa cipulumutso canga:

47 Ndiye Mulungu amene andibwe, zerera cilango, Nandigonjetsera mitundu ya anthu.

48 Andipulumutsa kwa adani anga: Inde mundikweza pa iwo akundiukira ine: Mundikwatula kwa munthu waciwawa.

49 Cifukwa cace Yehova ndidzakuyamikani mwa amitundu, Ndipo dzina lanu ndidzaliyimbira.

50 Alanditsa mfumu yace ndi cipulumutso cacikuru: Nacitira cifundo wodzozedwa wace, Davide, ndi mbumba yace, ku nthawi zonse.

19

1 Zakumwamba zimalalikira ulemerero wa Mulungu; Ndipo thambo lionetsa nchito ya manja ace.

2 Usana ndi usana ucurukitsa mau, Ndipo usiku ndi usiku uonetsa nzeru.

3 Palibe cilankhulidwe, palibe mau; Liu lao silimveka.

4 Muyeso wao wapitirira pa dziko lonse lapansi, Ndipo mau ao ku malekezero a m'dziko muli anthu. Iye anaika hema la dzuwa m'menemo,

5 Ndipo liri ngati mkwati wakuturuka m'cipinda mwace, Likondwera ngati ciphona kuthamanga m'njira.

6 Kuturuka kwace lituruka kolekezera thambo, Ndipo kuzungulira kwace lifikira ku malekezero ace: Ndipo kulibe kanthu kobisalira kutentha kwace.

7 Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo; Mboni za Yehova ziri zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru;

8 Malangizo a Yehova ali olungama, akukondweretsa mtima: Malamulo a Yehova ali oyera, akupenyetsa maso.

9 Kuopa Yehova kuli mbe, kwakukhalabe nthawi zonse: Maweruzo a Yehova ali oona, alungama konse konse.

10 Ndizo zifunika koposa golidi, inde, golidi wambiri woyengetsa: Zizuna koposa uci ndi zakukha za zisa zace,

11 Ndiponso kapolo wanu acenjezedwa nazo: M'kuzisunga izo muli mphotho yaikuru.

12 Adziwitsa zolowereza zace ndani? Mundimasule kwa zolakwa zobisika.

13 Ndiponso muletse kapolo wanu pa zodzitama; Zisacite ufumu pa ine: pamenepo ndidzakhala wangwiro, Ndi wosacimwa colakwa cacikuru.

14 Mau a m'kamwa mwanga ndi maganizo a m'mtima wanga abvomerezeke pamaso panu, Yehova, thanthwe langa, ndi Mombolo wanga,

20

1 Yehova akubvomereze tsiku la nsautso; Dzina la Mulungu wa Yakobo likuike pamsanje;

2 Likutumizire thandizo loturuka m'malo oyera, Ndipo likugwirizize kucokera m'Ziyoni;

3 Likumbukile zopereka zako zonse, Lilandire nsembe yako yopsereza;

4 Likupatse ca mtima wako, Ndipo likwaniritse upo wako wonse.

5 Tidzapfuula mokondwera mwa cipulumutso canu, Ndipo m'dzina la Mulungu wathu tidzakweza mbendera: Yehova akwaniritse mapempho ako onse.

6 Tsopano ndidziwa kuti Yehova apulumutsa wodzozedwa wace; Adzambvomereza m'Mwamba mwace moyera Ndi mphamvu ya cipulumutso ca dzanja lace lamanja.

7 Ena atama magareca, ndi ena akavalo: Koma ife tidzachula dzina la Yehova Mulungu wathu.

8 Iwowa anagonieka, nagwa: Koma ife tauka, ndipo takhala ciriri.

9 Yehova, pulumutsani, Mfumuyo atibvomereze tsiku lakuitana ife.

21

1 Yehova, adzasekera mfumu mu mphamvu yanu; Adzakondwera kwakukuru m'cipulumutso canu!

2 Mwampatsa iye cikhumbo ca mtimawace, Ndipo simunakana pempho la milomo yace.

3 Pakuti mumkumika iye ndi madalitso okoma: Muika korona wa golidi woyengetsa pamutu pace.

4 Anakupemphani moyo, mwampatsa iye; Mwamtalikitsira masiku ku nthawi za nthawi.

5 Ulemerero wace ngwaukuru mwa cipulumutso canu: Mumcitira iye ulemu ndi ukulu.

6 Pakuti mumuikira madalitso ku nthawi zonse; Mumkondweretsa ndi cimwemwe pankhope panu.

7 Pakuti mfumu akhulupirira Yehova, Ndipo mwa cifundo ca Wam'mwambamwamba sadzagwedezeka iye,

8 Dzanja lanu lidzapeza adani anu onse: Dzanja lanu lamanja lidzapeza iwo akuda Inu.

9 Mudzawaika ngati ng'anjo yamoto pa nyengo ya mkwiyo wanu. Yehova adzawatha m'kukwiya kwace, Ndipo moto udzawanyeketsa.

10 Mudzaziononga zobala zao kuzicotsa pa dziko lapansi, Ndi mbeu zao mwa ana a anthu.

11 Pakuti anakupangirani coipa: Anapangana ciwembu, osakhoza kucicita.

12 Pakuti mudzawabweza m'mbuyo, Popiringidza m'nsinga zanu pankhope pao,

13 Kwezekani, Yehova, mu mphamvu yanu: Potero tidzayimba ndi kulemekeza cilimbiko canu.

22

1 Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine? Mukhaliranji kutali kwa cipulumutso canga, ndi kwa mau a kubuula kwanga?

2 Mulungu wanga, ndiitana usana, koma simubvomereza; Ndipo usiku, sindikhala cete.

3 Koma Inu ndinu woyera, Wakukhala m'malemekezo a Israyeli.

4 Makolo athu anakhulupirira Inu: Anakhulupirira, ndipo munawalanditsa.

5 Anapfuula kwa Inu, napulumutsidwa: Anakhulupita Inu, ndipo sanacita manyazi.

6 Koma ine ndine nyongolotsi, si munthu ai: Cotonza ca anthu, ndi wonyozedwa ndi anthu.

7 Onse akundipenya andiseka: Akwenzula, apukusa mutu, nati,

8 Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa, Amlanditse tsopano popeza akondwera naye.

9 Pakuti Inu ndinu wondibadwitsa: Wondikhulupiritsa pokhala ine pa bere la mai wanga.

10 Cibadwire ine anandisiyira Inu: Kuyambira kwa mai wanga Mulungu wanga ndinu.

11 Musandikhalire kutali; pakuti nsautso iri pafupi: Pakuti palibe mthandizi.

12 Ng'ombe zamphongo zambiri zandizinga: Mphongo zolimba za ku Basana zandizungulira,

13 Andiyasamira m'kamwa mwao, Ngati mkango wozomola ndi wobangula.

14 Ndathiridwa pansi monga madzi, Ndipo mafupa anga onse anaguluka: Mtima wanga ukunga sera; Wasungunuka m'kati mwa matumbo anga,

15 Mphamvu yanga yauma ngati phale; Ndi lilime langa likangamira ku nsaya zanga; Ndipo mwandifikitsa ku pfumbi la imfa.

16 Pakuti andizinga agaru: Msonkhano wa oipa wanditsekereza; Andiboola m'manja anga ndi m'mapazi anga.

17 Ndikhoza kuwerenga mafupa anga onse; Iwo ayang'ana nandipenyetsetsa ine:

18 Agawana zobvala zanga, Nalota maere pa malaya anga,

19 Koma Inu, Yehova, musakhale kutari; Mphamvu yanga Inu, mufulumire kundithandiza.

20 Landitsani moyo wanga kulupanga; Wokondedwa wanga ku mphamvu ya garu,

21 Ndipulumutseni m'kamwa mwa mkango; Inde mwandiyankha ine ndiri pa nyanga za njati,

22 Ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga: Pakati pa msonkhano ndidzakulemekezani.

23 Inu akuopa Yehova, mumlemekeze; Inu nonse mbumba ya Yakobo, mumcitire ulemu; Ndipo mucite mantha ndi Iye, inu nonse mbumba ya Israyeli.

24 Pakuti sanapeputsa ndipo sananyansidwa ndi zunzo la wozunzika; Ndipo sanambisira nkhope yace; Koma pompfuulira Iye, anamva.

25 Lemekezo langa lidzakhala la Inu mu msonkhano waukuru: Zowinda zanga ndidzazicita pamaso pa iwo akumuopa Iye.

26 Ozunzika adzadya nadzakhuta: Adzayamika Yehova iwo amene amfuna: Ukhale moyo mtima wako nthawi zonse.

27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukila nadzatembenukira kwa Yehova: Ndipo mafuko onse a amitundu adzagwadira pamaso panu.

28 Pakuti ufumuwo ngwa Yehova; Iye acita ufumu mwa amitundu.

29 Onenepa onse a pa dziko lapansi adzadya nadzagwadira: Onse akutsikira kupfumbi adzawerama pamaso pace, Ndi iye amene sadziwa kusunga moyo wace.

30 Mbumba ya anthu idzamtumikira; Kudzanenedwa za Ambuye ku mibadwo yakudza.

31 Iwo adzadza nadzafotokozera cilungamo cace Kwa anthu akadzabadwa, kuti Iye anacicita.

23

1 Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.

2 Andigonetsa ku busa lamsipu: Anditsogolera ku madzi ndikha.

3 Atsitsimutsa moyo wanga; Anditsogolera m'mabande a cilungamo, cifukwa ca dzina lace.

4 Inde, ndingakhale ndiyenda m'cigwa ca mthunzi wa Imfa, Sindidzaopa coipa; pakuti Inu muli ndi ine: Cibonga canu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine,

5 Mundiyalikira gome pamaso panga m'kuona kwa adani anga: Mwandidzoza mutu wanga mafuta; cikho canga cisefuka.

6 Inde ukoma ndi cifundo zidzanditsata masiku onse a moyo wanga: Ndipo ndidzakhala m'nyumba ya Yehova masiku onse.

24

1 Dziko lapansi nla Yehova ndi zodzala zace zomwe, Dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhala m'mwemo.

2 Pakuti Iye analimanga pazinyanja, Nalikhazika pamadzi.

3 Adzakwera ndani m'phiri la Yehova? Nadzaima m'malo ace oyera ndani?

4 Woyera m'manja, ndi woona m'mtima, ndiye; Iye amene sanakweza moyo wace kutsata zacabe, Ndipo salumbira monyenga,

5 Iye adzalandira dalitso kwa Yehova, Ndi cilungamo kwa Mulungu wa cipulumutso cace.

6 Uwu ndi mbadwo wa iwo akufuna Iye, Iwo akufuna nkhope yanu, Mulungu wa Yakobo.

7 Weramutsani mitu yanu, zipata inu; Ndipo kwezekani inu, zitseko zosatha: Kuti Mfumu ya ulemerero ilowe.

8 Mfumu imene ya ulemerero ndani? Yehova wamphamvu ndi wolimba, Yehova wolimba kunkhondo.

9 Weramutsani mitu yanu, zipata inu; Inde weramutsani, zitseko zosatha inu, Kuti Mfumu ya ulemerero ilowe.

10 Mfumu imene ya ulemerero ndani? Yehova wa makamu makamu, Ndiye Mfumu ya ulemerero.

25

1 Ndikweza moyo wanga kwa Inu, Yehova.

2 Mulungu wanga, ndakhulupirira Inu, Ndisacite manyazi; Adani anga asandiseke ine.

3 Inde, onse akuyembekezera Inu sadzacita manyazi Adzacita manyazi iwo amene acita monyenga kopanda cifukwa.

4 Mundidziwitse njira zanu, Yehova; Mundiphunzitse mayendedwe anu.

5 Munditsogolere m'coonadi canu, ndipo mundiphunzitse; Pakuti Inu ndinu Mulungu wa cipulumutso canga; Inu ndikuyembekezerani tsiku lonseli.

6 Kumbukilani, Yehova, nsoni zanu ndi cifundo canu; Pakuti izi nza kale lonse,

7 Musakumbukile zolakwa za ubwana wanga kapena zopikisana nanu: Mundikumbukile monga mwa cifundo canu, Cifukwa ca ubwino wanu, Yehova.

8 Yehova ndiye wabwino ndi wolunjika mtima: Cifukwa cace adzaphunzitsa olawa za njira.

9 Adzawatsogolera ofatsa m'ciweruzo: Ndipo adzaphunzitsa ofatsa njira yace.

10 Mayendedwe onse a Yehova ndiwo cifundo ndi coonadi, Kwa iwo akusunga pangano lace ndi mboni zace.

11 Cifukwa ca dzina lanu, Yehova, Ndikhululukireni kusakaza kwanga, pakuti ndiko kwakukuru.

12 Munthuyo wakuopa Yehova ndani? Adzamlangiza iye njira adzasankheyo.

13 Moyo wace udzakhala mokoma; Ndi mbumba zace zidzalandira dziko lapansi.

14 Cinsinsi ca Yehova ciri kwa iwo akumuopa Iye; Ndipo adzawadziwitsa pangano lace.

15 Maso anga alinga kwa Yehova kosaleka; Pakuti Iye adzaonjola mapazi anga m'ukonde.

16 Ceukirani ine ndipo ndicitireni cifundo; Pakuti ndiri woungumma ndi wozunzika.

17 Masautso a mtima wanga akula: Munditurutse m'zondipsinja.

18 Penyani mazunzo anga ndi zabvuta zanga; Ndipo khululukirani zolakwa zanga zonse.

19 Penyani adani anga, popeza acuruka; Ndipo andida ndi udani waciwawa.

20 Sungani moyo wanga, ndilanditseni, Ndisakhale nao manyazi, pakuti ndakhulupirira Inu.

21 Ungwiro ndi kuongoka mtima zindisunge, Pakuti ndayembekezera Inu.

22 Ombolani Israyeli, Mulungu, M'masautso ace onse.

26

1 Mundiweruze, Yehova, pakuti ndayenda m'ungwiro wanga: Ndipo ndakhulupirira Yehova, sindidzaterereka.

2 Mundiyesere, Yehova, ndipo mundisunthe; Yeretsani imso zanga ndi mtima wanga.

3 Pakuti cifundo canu ciri pamaso panga; Ndipo ndayenda m'coona canu.

4 Sindinakhala pansi ndi anthu acabe; Kapena kutsagana nao anthu otyasika.

5 Ndidana nao msonkhano wa ocimwa, Ndipo sindidzakhala nao pansi ocita zoipa.

6 Ndidzasamba manja anga mosalakwa; Kuti ndizungulire guwa la nsembe lanu, Yehova:

7 Kuti ndimveketse mau a ciyamiko, Ndi kulalikira nchito zanu zonse zozizwa.

8 Yehova, ndikonda cikhalidwe ca nyumba yanu, Ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.

9 Musandicotsere mzimu wanga pamodzi ndi olakwa, Kapena moyo wanga pamodzi ndi anthu okhetsa mwazi:

10 Amene m'manja mwao muli mphulupulu, Ndi dzanja lao lamanja ladzala ndi zokometsera mlandu.

11 Koma ine, ndidzayenda m'ungwiro wanga; Mundiombole, ndipo ndicitireni cifundo.

12 Phazi langa liponda pacidikha: M'masonkhano ndidzalemekeza Yehova.

27

1 Yehova ndiye kuunika kwanga ndi cipulumutso canga; ndidzaopa yani? Yehova ndiye mphamvu ya moyo wanga; ndidzacita mantha ndi yani?

2 Pondifika ine ocita zoipa kudzadya mnofu wanga, Inde akundisautsa ndi adani anga, anakhumudwa iwo nagwa.

3 Lingakhale gulu la ankhondo limanga misasa kuti andithyole, Mtima wanga sungacite mantha: Ingakhale nkhondo ikandiukira, Nde pomweponso ndidzakhulupira,

4 Cinthu cimodzi ndinacipempha kwa Yehova, ndidzacilondola ici: Kuti ndikhalitse m'nyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, Kupenya kukongola kwace kwa Yehova ndi kufunsitsa m'Kacisi wace.

5 Cifukwa kuti pa dzuwa la tsoka Iye adzandibisa mumsasa mwace: Adzandibisa m'tsenjezi mwa cihema cace; Pathanthwe adzandikweza.

6 Ndipo tsopano mutu wanga udzakwezeka pamwamba pa adani anga akundizinga; Ndipo ndidzapereka m'cihema mwace nsembe za kupfuula mokondwera; Ndidzayimba, inde, ndidzayimbira Yehova zomlemekeza.

7 Imvani, Yehova, liu langa popfuula ine: Mundicitirenso cifundo ndipo mundibvomereze.

8 Pamene munati, Punani nkhope yanga; mtima wanga unati kwa Inu: Nkhope yanu, Yehova, ndidzaifuna.

9 Musandibisire ine nkhope yanu; Musacotse kapolo wanu ndi kukwiya: Inu munakhala thandizo langa; Musanditaye, ndipo musandisiye Mulungu wa cipulumutso canga,

10 Pakuti wandisiya atate wanga ndi amai wanga, Koma Yehova anditola.

11 Mundiphunzitse njira yanu, Yehova, Munditsogolere pa njira yacidikha, Cifukwa ca adani anga,

12 Musandipereke ku cifuniro ca akundisautsa; Cifukwa zinandiukira mboni zonama ndi iwo akupumira zaciwawa.

13 Ndikadapanda kukhulupirira kuti ndikaone ubwino wa Yehova M'dziko la amoyo, ndikadatanil

14 Yembekeza Yehova: Limbika, ndipo Iye adzalimbitsa mtima wako; Inde, yembekeza Yehova.

28

1 Kwa Inu, Yehova, ndidzapfuulira; Thanthwe langa, musandikhalire ngati wosamva: Pakuti ngati munditontholera ine, Ndidzafanana nao iwo akutsikira kumanda.

2 Mverani mau a kupemba kwanga, pamene ndilirira Inu, Pamene ndikweza manja anga kuloza ponenera panu poyera.

3 Musandikoke kundicotsa pamodzi ndi oipa, Ndi ocita zopanda pace; Amene alankhula zamtendere ndi anansi ao, Koma mumtima mwao muli coipa.

4 Muwapatse monga mwa nchito zao, ndi monga mwa coipa cocita iwo: Muwapatse monga mwa macitidwe a manja ao; Muwabwezere zoyenera iwo.

5 Pakuti sasamala nchito za Yehova, Kapena macitidwe a manja ace, Adzawapasula, osawamanganso.

6 Wodalitsika Yehova, Pakuti adamva mau a kupemba kwanga.

7 Yehova ndiye mphamvu yanga, ndi cikopa canga; Mtima wanga wakhulupirira Iye, ndipo anandithandiza: Cifukwa cace mtima wanga ukondwera kwakukuru; Ndipo ndidzamyamika nayo Nyimbo yanga.

8 Yehova ndiye mphamvu yao, Inde mphamvu ya cipulumutso ca wodzozedwa wace.

9 Pulumutsani anthu anu, ndi kudalitsa colandira canu: Muwawetenso, ndi kuwanyamula nthawi zonse.

29

1 Perekani kwa Yehova, inu ana a amphamvu, Perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

2 Perekani kwa Yehova ulemerero wa dzina lace: Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa.

3 Liu la Yehova liri pamadzi; Mulungu wa ulemerero agunda, Ndiye Yehova pa madzi ambiri.

4 Liu la Yehova ndi lamphamvu; Liu la Yehova ndi lalikurukuru.

5 Liu la Yehova lithyola mitengo yamkungudza; Inde Yehova athyola mikungudza ya ku Lebano.

6 Aitumphitsa monga mwana wa ng'ombe; Lebano ndi Sirio monga msona wa njati.

7 Liu la Yehova ligawa malawi a moto.

8 Liu la Yehova ligwedeza cipululu; Yehova agwedeza cipululu ca Kadese.

9 Liu la Yehova liswetsa nyama zazikazi, Ndipo lipulula nkhalango: Ndipo m'Kacisi mwace zonse ziri m'mwemo zimati, Ulemerero:

10 Yehova anakhala pa Cigumula: Inde Yehova akhala mfumu ku nthawi yomka muyaya.

11 Yehova adzapatsa anthu ace mphamvu: Yehova adzadalitsa anthu ace ndi mtendere.

30

1 Ndidzakukwezani, Yehova; pakuti mwandinyamutsa, Ndipo simunandikondwetsera adani anga,

2 Yehova, Mulungu wanga, Ndinapfuulira kwa Inu, ndipo munandiciritsa.

3 Yehova munabweza moyo wanga kumanda: Munandisunga ndi moyo, kuti ndingatsikire kudzenje.

4 Yimbirani Yehova, inu okondedwa ace, Ndipo yamikani pokumbukila ciyero cace.

5 Pakuti mkwiyo wace ukhala kanthawi kokha; Koma kuyanja kwace moyo wonse: Kulira kucezera, Koma mamawa kuli kupfuula kukondwera.

6 Ndipo ine, ndinanena m'phindu langa, Sindidzagwedezeka nthawi zonse.

7 Inu, Yehova, munakhazikitsa phiri langa ndi kuyanja kwanu: Munabisa nkhope yanu; ndinaopa.

8 Ndinapfuulira kwa Inu, Yehova; Kwa Yehova ndinapemba:

9 M'mwazi mwanga muli phindu lanji, potsikira ine kudzenje? Ngati pfumbi lidzayamika Inu? ngati lidzalalikira coonadi canu?

10 Mverani, Yehova, ndipo ndicitireni cifundo: Yehova, mundithandize ndi Inu.

11 Munasanduliza kulira kwanga kukhale kusekera; Munandibvula ciguduli canga, ndipo munandibveka cikondwero:

12 Kuti ulemu wanga uyimbire Inu, wosakhala cete. Yehova Mulungu wanga, ndidzakuyamikani nthawi zonse.

31

1 Ndakhulupirira Inu, Yehova, ndikhale wopanda manyazi nthawi zonse: Mwa cilungamo canu ndipulumutseni ine.

2 Mundicherere khutu lanu; ndipulumutseni msanga: Mundikhalire ine thanthwe lolimba, nyumba yamalinga yakundisunga.

3 Pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa; Ndipo cifukwa ca dzina lanu ndiyendetseni bwino, ndipo nditsogolereni.

4 Mundionjole m'ukonde umene anandichera mobisika. Pakuti Inu ndinu mphamvu yanga.

5 Ndipereka mzimu wanga m'dzanja lanu: Mwandiombola, Inu Yehova, Mulungu wa coonadi.

6 Ndikwiya nao iwo akusamala zacabe zonama: Koma ndikhulupirira Yehova.

7 Ndidzakondwera ndi kusangalala m'cifundo canu: Pakuti mudapenya zunzo langa; Ndipo mudadziwa mzimu wanga mu nsautso yanga:

8 Ndipo simunandipereka m'dzanja la mdani; Munapondetsa mapazi anga pali malo.

9 Mundicitire cifundo, Yehova, pakuti ndasautsika ine: Diso langa, mzimu wanga, ndi mimba yanga, zapuwala ndi mabvuto,

10 Pakuti moyo wanga watha ndi cisoni, ndi zaka zanga zatha ndi kuusa moyo: Mphamvu yanga yafoka cifukwa ca kusakaza kwanga, ndi mafupa anga apuwala.

11 Ndakhala cotonza cifukwa ca akundisautsa onse, Inde, koposa kwa anansi anga; ndipo anzanga andiyesa coopsa: Iwo akundipenya pabwalo anandithawa.

12 Ndaiwalika m'mtima monga wakufa: Ndikhala monga cotengera cosweka.

13 Pakuti ndamva ugogodi wa ambiri, Mantha andizinga: Pondipangira ciwembu, Anatsimikiza mtima kulanda moyo wanga.

14 Koma ine ndakhulupirira Inu, Yehova: Ndinati, Inu ndinu Mulungu wanga,

15 Nyengo zanga ziri m'manja mwanu: Mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.

16 Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu: Mundipulumutse ndi cifundo canu.

17 Yehova, musandicititse manyazi; pakuti ndapfuulira kwa Inu: Oipa acite manyazi, atonthole m'manda.

18 Ikhale yosalankhula milomo ya mabodza, Imene imalankhula mwacipongwe pa olungama mtima, Ndi kudzikuza ndi kunyoza.

19 Ha! kukoma kwanu ndiko kwakukuru nanga, kumene munasungira iwo akuopa Inu, Kumene munacitira iwo akukhulupirira Inu, pamaso pa ana a anthu!

20 Pobisalira pamaso panu mudzawabisa kwa ciwembu ca munthu: Mudzawabisa iwo mumsasa kuti muwalanditse pa kutetana kwa malilime.

21 Wolemekezeka Yehova: Pakuti anandicitira cifundo cace codabwiza m'mudzi walinga.

22 Ndipo ine, pakutenga nkhawa, ndinati, Ndadulidwa kundicotsa pamaso panu: Komatu munamva mau a kupemba kwanga pamene ndinapfuulira kwa Inu.

23 Kondani Yehova, Inu nonse okondedwa ace: Yehova asunga okhulupirika, Ndipo abwezera zocuruka iye wakucita zodzitama.

24 Limbikani, ndipo Iye adzalimbitsa mtima wanu, Inu nonse akuyembekeza Yehova.

32

1 Wodala munthuyo wokhululukidwa chimo lace; Wokwiriridwa coipa cace.

2 Wodala munthuyu Yehova samwerengera mphulupulu zace; Ndimo mumzimu mwace mulibe cinyengo.

3 Pamene ndinakhala cete mafupa anga anakalamba Ndi kubuula kwanga tsiku lonse.

4 Cifukwa usana ndi usiku dzanja lanu linandilemera ine; Uwisi wanga unasandulika kuuma kwa malimwe.

5 Ndinabvomera coipa canga kwa Inu; Ndipo mphulupulu yanga sindinaibisa. Ndinati, Ndidzaululira Yehova macimo anga; Ndipo munakhululukira coipa ca kulakwa kwanga.

6 Cifukwa cace oyera mtima onse apemphere kwa Inu, Pa nthawi ya kupeza Inu: Indetu pakusefuka madzi akuru Sadzamfikira iye.

7 Inu ndinu mobisalira mwanga; M'nsautso mudzandisunga; Mudzandizinga ndi Nyimbo za cipulumutso.

8 Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo; Ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang'ana iwe.

9 Musakhale monga kavalo, kapena ngati buru, wopanda nzeru: Zomangira zao ndizo cam'kamwa ndi capamutu zakuwakokera, Pakuti ukapanda kutero sadzakuyandikiza.

10 Zisoni zambiri zigwera woipa: Koma cifundo cidzamzinga iye wakukhulupirira Yehova.

11 Sekerani mwa Yehova, ndimo kondwerani inu olungama mtima; Ndipo pfuulani mokondwera nonsenu oongoka mtima.

33

1 Pfuulani mokondwera mwa Yehova, inu olungama mtima: Oongoka mtima ayenera kulemekeza.

2 Yamikani Yehova ndi zeze: Myimbireni ndi cisakasa ca zingwe khumi.

3 Mumyimbire Iye Nyimbo yatsopano; Muyimbe mwaluso kumveketsa mau.

4 Pakuti mau a Yehova ali olunjika; Ndi nchito zace zonse zikhulupirika.

5 Iye ndiye wakukonda cilungamo ndi ciweruzo: Dziko lapansi ladzala ndi cifundo ca Yehova.

6 Zakumwamba zinalengedwa ndi mau a Yehova; Ndipo ndi mpweya wa m'kamwa mwace khamu lao lonse.

7 Amaunjika madzi a m'nyanja monga mulu: Amakundika zakudya mosungiramo.

8 Dziko lonse lapansi liope Yehova: Ponse pali anthu acite mantha cifukwa ca Iye,

9 Pakuti ananena, ndipo cinacitidwa; Analamulira, ndipo cinakhazikika.

10 Yehova aphwanya upo wa amitundu: Asandutsa cabe zolingirira za mitundu ya anthu.

11 Ciweruzo ca Yehova cikhazikika cikhazikikire, Zolingirira za m'mtima mwace ku mibadwo mibadwo.

12 Wodalitsika mtundu wa anthu umene Yehova ndiye Mulungu wao; Mtundu womwe anausankha ukhale colandira ca iye yekha.

13 Yehova apenyerera m'mwamba; Aona ana onse a anthu.

14 M'malo akhalamo Iye, amapenya pansi Pa onse akukhala m'dziko lapansi;

15 Iye amene akonza mitima ya iwo onse, Amene azindikira zocita zao zonse.

16 Palibe mfumu yoti gulu lalikuru limpulumutsa: Mphamvu yaikuru siicilanditsa ciphona,

17 Kavalo safikana kupulumuka naye: Cinkana mphamvu yace njaikuru sapulumutsa.

18 Taonani, diso la Yehova liri pa iwo akumuopa Iye, Pa iwo akuyembekeza cifundo cace;

19 Kupulumutsa moyo wao kwa imfa, Ndi kuwasunga ndi moyo m'nyengo ya njala.

20 Moyo wathu walindira Yehova: Iye ndiye thandizo lathu ndi cikopa cathu.

21 Pakuti mtima wathu udzakondwera mwa Iye, Cifukwa takhulupirira dzina lace loyera.

22 Yehova, cifundo canu cikhale pa ife, Monga takuyembekezani Inu.

34

1 Ndidzalemekeza Yehova nyengo zonse; Kumlemekeza kwace kudzakhala m'kamwa mwanga kosalekeza.

2 Moyo wanga udzatamanda Yehova; Ofatsa adzakumva nadzakondwera.

3 Bukitsani pamodzi ndine ukuru wa Yehova, Ndipo tikweze dzina lace pamodzi.

4 Ndinafuna Yehova ndipo anandibvomera, Nandlianditsa m'mantha anga Onse.

5 Iwo anayang'ana Iye nasanguruka; Ndipo pankhope pao sipadzacita manyazi,

6 Munthu uyu wozunzika anapfuula, ndipo Yehova anamumva, Nampulumutsa m'masautso ace onse.

7 Mngelo wa Yehova azinga kuwacinjiriza iwo akuopa Iye, Nawalanditsa iwo.

8 Talawani, ndipo onani kuti Yehova ndiye wabwino; Wodala munthuyo wakukhulupirira Iye.

9 Opani Yehova, inu oyera mtima ace; Cifukwa iwo akumuopa Iye sasowa.

10 Misona ya mkango isowa nimva njala: Koma iwo akufuna Yehova sadzasowa kanthu kabwino.

11 Idzani ananu ndimvereni ine: Ndidzakulangizani zakumuopa Yehova.

12 Munthu wokhumba moyo ndani, Wokonda masiku, kuti aone zabwino?

13 Uletse lilime lako lisachule zoipa, Ndipo milomo yako isalankhule cinyengo.

14 Pfutuka pazoipa, nucite zabwino, Funa mtendere ndi kuulondola.

15 Maso a Yehova ali pa olungama mtima, Ndipo makutu ace achereza kulira kwao.

16 Nkhopeya Yehovaitsutsananao akucita zoipa, Kudula cikumbukilo cao pa dziko lapansi.

17 Iwowo anaitana, ndipo Yehova anawamva, Nawalanditsa ku masautso ao onse.

18 Yehova ali pafupi ndi iwo a mtimawosweka, Apulumutsa iwo a mzimu wolapadi,

19 Masautso a wolungama mtima acuruka: Koma Yehova amlanditsa mwa onsewa.

20 Iye asunga mafupa ace onse: Silinatyoka limodzi lonse.

21 Mphulupulu idzamupha woipa: Ndipo adzawatsutsa kumlandu iwo akudana naye wolungama.

22 Yehova aombola moyo wa anyamata ace, Ndipo sadzawatsutsa kumlandu onse akukhulupirira Iye.

35

1 Tsutsanani nao iwo akutsutsana nane, Yehova: Limbanani nao iwo akulimbana nane.

2 Gwirani cikopa cocinjiriza, Ukani kundithandiza.

3 Sololani nthungo, ndipo muwatsekerezere kunjira akundilondola: Nenani ndi moyo wanga, Cipulumutso cako ndine.

4 Athe nzeru nacite manyazi iwo akufuna moyo wanga: Abwezedwe m'mbuyo nasokonezeke iwo akundipangira ciwembu.

5 Akhale monga mungu kumphepo, Ndipo mngelo wa Yehova awapitikitse.

6 Njira yao ikhale ya mdima ndi yoterera, Ndipo mngelo wa Yehova awalondole.

7 Pakuti anandichera ukonde wao m'mbunamo kopanda cifukwa, Anakumbira moyo wanga dzenje kopanda cifukwa.

8 Cimgwere modzidzimutsa cionongeko; Ndipo ukonde wace umene anaucha umkole yekha mwini: Agwemo, naonongeke m'mwemo.

9 Ndipo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova: Udzasekera mwa cipulumutso cace.

10 Mafupa anga onse adzanena, Yehova, afanana ndi Inu ndani, Wakulanditsa wozunzika kwa iye amene amposa mphamvu, Ndi wozunzika ndi waumphawi kwa iye amfunkhira?

11 Mboni za ciwawa ziuka, Zindifunsa zosadziwa ine.

12 Andibwezera coipa m'malo mwa cokoma, Inde, asaukitsa moyo wanga.

13 Koma ine, pakudwala iwowa, cobvala canga ndi ciguduli: Ndinazunza moyo wanga ndi kusala; Ndipo pemphero langa linabwera ku cifuwa canga.

14 Ndakhala ine monga ngad iye anali bwenzi langa, kapena mbale wanga: Polira ndinaweramira pansi, monga munthu wakulira maliro amai wace.

15 Ndipo pakutsimphina ine anakondwera, nasonkhana pamodzi: Akundipanda anandisonkhanira; ndipo sindinacidziwa: Ananding'amba osaleka:

16 Pakati pa onyodola pamadyerero, Anandikukutira mano.

17 Ambuye, mudzapenyerabe nthawi yanji? Bwezani moyo wanga kwa zakundiononga zao, Wanga wa wokha kwa misona ya mkango.

18 Ndidzakuyamikanimumsonkhano waukuru: M'cikhamu ca anthu ndidzakulemekezani.

19 Adani anga asandikondwerere ine monyenga; Okwiya nane kopanda cifukwa asanditsinzinire.

20 Pakuti salankhula zamtendere: Koma apangira ciwembu odekha m'dziko.

21 Ndipo andiyasamira m'kamwa mwao; Nati, Hede, Hede, diso lathu lidacipenya.

22 Yehova, mudacipenya; musakhale cete: Ambuye, musakhale kutali ndi ine.

23 Galamukani, ndipo khalani maso kundiweruzira mlandu wanga, Mulungu wanga ndi Ambuye wanga,

24 Mundiweruze monga mwa cilungamo canu, Yehova Mulungu wanga; Ndipo asandisekerere ine.

25 Asanene mumtima mwao, Hede, momwemo! Asanene, Tammeza iye.

26 Acite manyazi, nadodome iwo akukondwera cifukwa ca coipa cidandigwera: Abvekeke ndi manyazi ndi kupunzika iwo akudzikuza pa ine.

27 Apfuule mokondwera nasangalale iwo akukondwera naco cilungamo canga: Ndipo anene kosalekeza, Abuke Yehova, Amene akondwera ndi mtendere wa mtumiki wace.

28 Ndipo lilime langa lilalikire cilungamo canu, Ndi lemekezo lanu tsiku lonse.

36

1 Colakwa ca woipayo cimati m'kati mwa mtima wanga, Palibe kuopa Mulungu pamaso pace.

2 Pakud adzidyoletsa yekha m'kuona kwace, Kuti anthu sadzacipeza coipa cace ndi kukwiya naco.

3 Mau a pakamwa pace ndiwo opanda pace ndi onyenga: Waleka kuzindikira ndi kucita bwino.

4 Alingirira zopanda pace pakama pace; Adziika panjira posad pabwino; Coipa saipidwa naco.

5 Yehova, m'mwambamuli cifundo canu; Coonadi canu cifikira kuthambo.

6 Cilungamo canu cikunga mapiri a Mulungu; Maweruzo anu akunga cozama cacikuru: Yehova, musunga munthu ndi nyama.

7 Ha! cifundo canu, Mulungu, ncokondedwadi! Ndipo ana a anthu athawira ku mthunzi wa mapiko anu.

8 Adzakhuta kwambiri ndi zonona za m'nyumba mwanu: Ndipo mudzawamwetsa mu mtsinje wa zokondweretsa zanu.

9 Pakuti citsime ca moyo ciri ndi Inu: M'kuunika kwanu tidzaona kuunika.

10 Tanimphitsani cifundo canu pa iwo akudziwa Inu; Ndi cilungamo canu pa oongoka mtima.

11 Phazi la akudzikuza lisandifikire ine, Ndi dzanja la oipa lisandicotse.

12 Pomwepo padagwera ocita zopanda pace: Anawalikha, ndipo sadzatha kuukanso.

37

1 Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa, Usacite nsanje cifukwa ca ocita cosalungama.

2 Pakuti adzawamweta msanga monga udzu, Ndipo adzafota monga msipu wauwisi.

3 Khulupirira Yehova, ndipo cita cokoma; Khala m'dziko, ndipo tsata coonadi.

4 Udzikondweretsenso mwa Yehova; Ndipo iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

5 Pereka njira yako kwa Yehova; Khulupiriranso Iye, adzacicita.

6 Ndipo adzaonetsa cilungamo cako monga kuunika, Ndi kuweruza kwako monga usana.

7 Khala cete mwa Yehova, numlindirire Iye: Usabvutike mtima cifukwa ca iye wolemerera m'njira yace, Cifukwa ca munthu wakucita ciwembu.

8 Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo: Usabvutike mtima ungacite coipa,

9 Pakuti ocita zoipa adzadulidwa: Koma iwo akuyembekeza Yehova, iwowa adzalandira dziko lapansi.

10 Katsala kanthawi ndipo woipa adzatha psiti: Inde, udzayang'anira mbuto yace, nudzapeza palibe.

11 Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi; Nadzakondwera nao mtendere wocuruka.

12 Woipa apangira ciwembu wolungama, Namkukutira mano.

13 Ambuye adzamseka: Popeza apenya kuti tsiku lace likudza.

14 Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao; Alikhe ozunzika ndi aumphawi, Aphe amene ali oongoka m'njira:

15 Lupanga lao lidzalowa m'mtima mwao momwe, Ndipo mauta ao adzatyoledwa.

16 Zocepa zace za wolungama zikoma Koposa kucuruka kwao kwa oipa ambiri.

17 Pakuti manja a oipa adzatyoledwa: Koma Yehova acirikiza olungama.

18 Yehova adziwa masiku a anthu angwiro: Ndipo cosiyira cao cidzakhala cosatha.

19 Sadzacita manyazi m'nyengo yoipa: Ndipo m'masiku a njala adzakhuta.

20 Pakuti oipa adzatayika, Ndipo adani ace a Yehova adzanga mafuta a ana a nkhosa: Adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.

21 Woipa akongola, wosabweza: Koma wolungama acitira cifundo, napereka.

22 Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi; Koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.

23 Yehova akhazikitsa mayendedwe a munthu; Ndipo akondwera nayo njira yace.

24 Angakhale akagwa, satayikiratu: Pakuti Yehova agwira dzanja lace.

25 Ndinali mwana ndipo ndakalamba: Ndipo sindinapenya wolungama wasiyidwa, Kapena mbumba zace zirinkupempha cakudya.

26 Tsiku lonse acitira cifundo, nakongoletsa; Ndipo mbumba zace zidalitsidwa.

27 Siyana naco coipa, nucite cokoma, Nukhale nthawi zonse.

28 Pakuti Yehova akonda ciweruzo, Ndipo sataya okondedwa ace: Asungika kosatha: Koma adzadula mbumba za oipa.

29 Olungama adzalandira dziko lapansi, Nadzakhala momwemo kosatha.

30 Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru, Ndi lilime lace linena ciweruzo.

31 Malamulo a Mulungu wace ali mumtima mwace; Pakuyenda pace sadzaterereka.

32 Woipa aunguza wolungama, Nafuna kumupha.

33 Yehova sadzamsiya m'dzanja lace: Ndipo sadzamtsutsa poweruzidwa iye.

34 Yembekeza Yehova, nusunge njira yace, Ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko: Pakudutidwa oipa udzapenya,

35 Ndapenya woipa, alikuopsa, Natasa monga mtengo wauwisi wanzika.

36 Koma anapita ndipo taona, kwati zi: Ndipo ndinampwaira osampeza.

37 Tapenya wangwiro, ndipo taona woongoka mtima! Pakuti ku matsiriziro ace a munthuyo kuti mtendere.

38 Koma olakwa adzaonongeka pamodzi: Matsiriziro a oipa adzadutidwa.

39 Koma cipulumutso ca olungama cidzera kwa Yehova, Iye ndiye mphamvu yao m'nyengo ya nsautso.

40 Ndipo Yehova awathandiza, nawalanditsa: Awalanditsa kwa oipa nawapulumutsa, Cifukwa kuti anamkhulupirira Iye,

38

1 Yehova, musandidzudzule ndi mkwiyo wanu: Ndipo musandilange moopsa m'mtima mwanu.

2 Pakuti mibvi yanu yandilowa, Ndi dzanja lanu landigwera.

3 Mumnofu mwanga mulibe camoyo cifukwa ca ukali wanu; Ndipo m'mafupa anga simuzizira, cifukwa ca colakwa canga.

4 Pakuti mphulupulu zanga zapitirira pamutu panga: Ndathodwa nazo monga ndi katundu wolemera.

5 Mabala anga anunkha, adaola, Cifukwa ca kupusa kwanga.

6 Ndapindika, ndawerama kwakukuru; Ndimayenda woliralira tsiku lonse.

7 Pakuti m'cuuno mwanga mutentha kwambiri; Palibe pamoyo m'mnofu mwanga,

8 Ndafoka ine, ndipo ndacinjizidwa: Ndabangula cifukwa ca kumyuka mtima wanga.

9 Ambuye, cikhumbo canga conse ciri pamaso panu; Ndipo kubuula kwanga sikubisika kwa Inu.

10 Mtima wanga ugundagunda, mphamvu yanga yacoka: Ndipo kuunika kwa maso anga, ndi iko komwe kwandicokera.

11 Ondikonda ndi anzanga apewa mliri wanga; Ndipo anansi anga aima patali.

12 Ndipo andichera misampha iwo akufuna moyo wanga; Ndipo iwo akuyesa kundicitira coipa alankhula zoononga, Nalingirira zonyenga tsiku lonse.

13 Koma ine, monga gonthi, sindimva; Ndipo monga munthu wosalankhula, sinditsegula pakamwa panga.

14 Inde ndikunga munthu wosamva, Ndipo m'kamwa mwanga mulibe makani.

15 Pakuti ndikuyembekezani Inu, Yehova; Inu mudzayankha, Ambuye Mulungu wanga.

16 Pakuti ndinati, Asakondwerere ine: Pakuterereka phazi langa, asadzikuze pa ine.

17 Ndafikana potsimphina; Ndipo cisoni canga ciri pamaso panga cikhalire.

18 Pakuti ndidzafotokozera mphulupulu yanga; Nditenga nkhawa cifukwa ca chimo langa.

19 Koma adani anga ali ndi moyo, nakhalandi mphamvu: Ndipo akundida kopanda cifukwa acuruka.

20 Ndipo iwo akubwezera coipa pa cabwino Atsutsana nane, popeza nditsata cabwino.

21 Musanditaye, Yehova: Mulungu wanga, musakhale kutali ndi ine.

22 Fulumirani kundithandiza, Ambuye, cipulumutso canga.

39

1 Ndinati, Ndidzasunga njira zanga, Kuti ndingacimwe ndi lilime langa: Ndidzasunga pakamwa panga ndi cam'kamwa, Pokhala woipa ali pamaso panga.

2 Ndinatonthola osanena mau, ndinakhala cete osalawa cokoma; Ndipo cisoni canga cinabuka.

3 Mtima wanga unatentha m'kati mwaine; Unayaka moto pakulingirira ine: Pamenepo ndinalankhula ndi lilime langa:

4 Yehova, mundidziwitse cimariziro canga, Ndi mawerengedwe a masiku anga ndi angati; Ndidziwe malekezero anga,

5 Onani, munaika masiku anga akhale monga kuyesa dzanja; Ndipo zaka zanga ziri ngati cabe pamaso panu: Indedi munthu ali yense angakhale wokhazikika, ali cabe konse.

6 Indedi munthu ayenda ngati mthunzi: Indedi abvutika cabe: Asonkhanitsa cuma, ndipo sadziwa adzacilandira ndani?

7 Ndipo tsopano, Ambuye, ndilindira ciani? Ciyembekezo canga ciri pa Inu.

8 Ndipulumutseni kwa zolakwa zangazonse: Musandiike ndikhale cotonza ca wopusa.

9 Ndinakhala du, sindinatsegula pakamwa panga; Cifukwa inu mudacicita.

10 Mundicotsere cobvutitsa canu; Pandithera ine cifukwa ca kulanga kwa dzanja lanu.

11 Pamene mulanga munthu ndi zomdzudzula cifukwa ca mphulupulu, Mukanganula kukongola kwace monga mumacita ndi kadzoce: Indedi, munthu ali yense ali cabe.

12 Imvani pemphero langa, Yehova, ndipo cherani khutu kulira kwanga; Musakhale cete pa misozi yanga: Pakuti ine ndine mlendo ndi Inu, Wosakhazikika, monga makolo anga onse.

13 Ndiloleni, kuti nditsitsimuke, Ndisanamuke ndi kukhala kuli zi.

40

1 Kuyembekeza ndayembekeza Yehova; Ndipo anandilola, namva kupfuula kwanga.

2 Ndipo anandikweza kunditurutsa m'dzenje la citayiko, ndi m'thope la pacithaphwi; Nandipondetsa pathanthwe, nakhazika mayendedwe anga.

3 Ndipo anapatsa Nyimbo yatsopano m'kamwa mwanga, cilemekezo ca kwa Mulungu wanga; Ambiri adzaciona, nadzaopa, Ndipo adzakhulupirira Yehova.

4 Wodala munthuyo wakuyesa Yehova wokhulupirika; Wosasamala odzikuza, ndi opatukira kubodza.

5 Inu, Yehova, Mulungu wanga, zodabwiza zanu mudazicita nzambiri, Ndipo zolingirira zanu za pa ife; Palibe wina wozifotokozera Inu; Ndikazisimba ndi kuzichula, Zindicurukira kuziwerenga.

6 Nsembe ndi copereka simukondwera nazo; Mwanditsegula makutu: Nsembe yopsereza ndi yamacimo simunapempha.

7 Pamenepo ndinati, Taonani, ndadza; M'buku mwalembedwa za Ine:

8 Kucita cikondwero canu kundikonda, Mulungu wanga; Ndipo malamulo anu ali m'kati mwamtima mwanga.

9 Ndalalikira cilungamo mu msonkano waukuru; Onani, sindidzaletsa milomo yanga, Mudziwa ndinu Yehova.

10 Cilungamo canu sindinacibisa m'kati mwamtima mwanga; Cikhulupiriko canu ndi cipulumutso canu ndinacinena; Cifundo canu ndi coonadi canu sindinacibisira msonkhano waukuru.

11 Inu Yehova, simudzandikaniza nsoni zanu: Cifundo canu ndi coonadi canu zindisunge cisungire.

12 Pakuti zoipa zosawerengeka zandizinga, Zocimwa zanga zandipeza kotero kuti sindikhoza kupenya; Ziposa tsitsi la mutu wanga, ndipo wandicokera mtima.

13 Ndikupemphani, Yehova, ndilanditseni: Fulumirani kudzandithandiza, Yehova.

14 Acite manyazi nadodome Iwo akulondola moyo wanga kuti auononge: Abwerere m'mbuyo, nacite manyazi iwo okondwera kundicitira coipa.

15 Apululuke, mobwezera manyazi ao Amene anena nane, Hede, hede.

16 Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu: Iwo akukonda cipulumutso canu asaleke kunena, Abuke Yehova.

17 Ndipo ine ndine wozunzika ndi waumphawi; Koma Ambuye andikumbukila ine: Inu ndinu mthandizi wanga, ndi mpulumutsi wanga: Musamacedwa, Mulungu wanga,

41

1 Wodala iye amene asamalira wosauka: Tsiku la tsoka Yehova adzampulumutsa:

2 Yehova adzamsunga, nadzamsunga ndi moyo, ndipo adzadalitsika pa dziko lapansi; Ndipo musampereke ku cifuniro ca adani ace.

3 Yehova adzamgwiriziza pa kama wodwalira; Podwala iye mukonza pogona pace,

4 Ndinati ine, Mundicitire cifundo, Yehova: Ciritsani mtima wanga; pakuti ndacimwira Inu.

5 Adani anga andinenera coipa, ndi kuti, Adzafa liti, ndi kutayika dzina lace?

6 Ndipo akadza kundiona wina angonena bodza; Mumtima mwace adzisonkhera zopanda pace: Akamka nayenda namakanena:

7 Onse akudana nane andinong'onezerana; Apangana condiipsa ine.

8 Camgwera cinthu coopsa, ati; Popeza ali gonire sadzaukanso.

9 Ngakhale bwenzi langa leni leni, amene ndamkhulupirira, ndiye amene adadyako mkate wanga, Anandikwezera cidendene cace.

10 Koma Inu, Yehova, mundicitire cifundo, ndipo mundiutse, Kuti ndiwabwezere.

11 Umo ndidziwa kuti mukondwera ndi ine, Popeza mdani wanga sandiseka.

12 Ndipo ine, mundigwirizize m'ungwiro wanga, Ndipo mundiike pankhope panu ku nthawi yamuyaya.

13 Wodalitsika Yehova, Mulungu wa Israyeli, Kucokera nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha. Amen, ndi Amen.

42

1 Monga nswala ipuma wefuwefu kukhumba mitsinje; Motero moyo wanga upuma wefuwefu kukhumba Inu, Mulungu.

2 Moyo wanga uli ndi ludzu la kwa Mulungu, la kwa Mulungu wamoyo: Ndikadze liti kuoneka pamaso pa Mulungu?

3 Misozi yanga yakhalangati cakudya canga, Usana ndi usiku; Pakunena iwo kwa ine dzuwa lonse, Mulungu wako ali kuti?

4 Ndizikumbukila izi ndipo nditsanulira moyo wanga m'kati mwa ine, Pakuti ndidafopita ndi unyinji wa anthu, Ndinawatsogolera ku nyumba ya Mulungu, ndi mau akuyimbitsa ndi kuyamika, Ndi unyinji wakusunga dzuwa lokondwera.

5 Udziweramiranji moyo wanga iwe? Ndi kuzingwa m'kati mwanga? Yembekeza Mulungu, pakuti ndidzamyamikanso Cifukwa ca cipulumutso ca nkhope yace.

6 Mulungu wanga, moyo wanga Udziweramira m'kati mwanga; Cifukwa cace ndikumbukila Inu m'dziko la Yordano, Ndi mu Ahermone, m'kaphiri ka Mizara.

7 Madzi akuya aitanizana ndi madzi akuya, Pa mkokomo wa matiti anu: Mafunde onse a nyondonyondo anandimiza ine.

8 Koma usana Yehova adzalamulira cifundo cace, Ndipo usiku Nyimbo yace idzakhala ndi ine. Inde pemphero la kwa Yehova wa moyowanga.

9 Ndidzati kwa Mulungu, thanthwe langa, mwandiiwala cifukwa ninji? Ndimayenderanji wakulira Cifukwa ca kundipsinja mdaniyo?

10 Adani anga andinyoza ndi kundityola mafupa anga; Pakunena ndine dzuwa lonse, Mulungu wako ali kuti?

11 Udziweramiranji moyo wanga iwe? Ndi kuzingwa m'kati mwanga? Yembekeza Mulungu: pakuti ndidzamlemekeza tsopanonso, Ndiye cipulumutso ca nkhope yanga ndi Mulungu wanga,

43

1 Mundiweruzire, Mulungu, ndipo mundinenere mlandu kwa anthu opanda cifundo: Mundilanditse kwa munthu wonyenga ndi wosalungama.

2 Pakuti Inu ndinu Mulungu wa mphamvu yanga; mwanditayiranji? Ndimayenderanji woliralira cifukwa ca kundipsinja mdani?

3 Tumizirani kuunika kwanu ndi coonadi canu zinditsogolere: Zindifikitse ku phiri lanu loyera, Kumene mukhala Inuko.

4 Kuti ndipite kufikira guwa la nsembe la Mulungu, Kufikira Mulungu wa cimwemwe canga ceniceni: Ndi kuti ndikuyamikeni ndi zeze, Mulungu, Mulungu wanga.

5 Udziweramiranji moyo wanga iwe? Ndi kuzingwa m'kati mwanga? Yembekeza Mulungu: pakuti ndidzamyamikanso, Ndiye cipulumutso ca nkhope yanga, ndi Mulungu wanga.

44

1 Mulungu, tidamva m'makutu mwathu, makolo athu anatisimbira, Za nchitoyo mudaicita masiku ao, masiku akale.

2 Inu munapitikitsa amitundu ndi dzanja lanu, koma iwowa munawaoka; Munasautsa mitundu ya anthu, ndipo munawaingitsa,

3 Pakuti sanalanda dziko ndi lupanga lao, Ndipo mkono wao sunawapulumutsa: Koma dzanja lanu lamanja, ndi mkono wanu, ndi kuunika kwa nkhope yanu. Popeza munakondwera nao,

4 Inu ndinu mfumu yanga, Mulungu: Lamulirani cipulumutso ca Yakobo.

5 Mwa Inu tidzakankhira pansi otsutsana nafe: M'dzina lanu tidzapondereza akutiukira ife.

6 Pakuti sinditama uta wanga, Ndipo lupanga langa silingandipulumutse.

7 Koma Inu munatipulumutsa kwa iwo akutsutsana nafe, Ndipo akudana nafe, mudawacititsa manyazi.

8 Mwa Mulungu tidzitamanda tsiku lonse, Ndipo dzina lanu tidzaliyamika kosatha.

9 Koma mwatitaya, ndi kutinyazitsa; Ndipo simuturuka nao makamu a nkhondo athu.

10 Mutibwereretsa kuthawa otisautsa: Ndipo akudana nafe adzifunkhira okha.

11 Mwatipereka ngati nkhosa zoyenera kuzidya; Ndipo mwatibalalitsa mwa amitundu.

12 Mugulitsa anthu anu kwacabe, Ndipo mtengo wace simupindula nao.

13 Mutisandutsa cotonza kwa anzathu, Ndi coseketsa ndi colalatitsa iwo akutizinga.

14 Mutiika tikhale onyozeka mwa amitundu, Ndi kuti anthu atipukusire mitu.

15 Tsiku lonse cimpepulo canga cikhala pamaso panga, Ndipo manyazi a pankhope panga andikuta.

16 Cifukwa ca mau a wotonza wocitira mwano; Cifukwa ca mdani ndi wobwezera cilango,

17 Zonsezi zatigwera; koma sitinakuiwalani, Ndipo sitinacita monyenga m'pangano lanu.

18 Mtima wathu sunabwerera m'mbuyo, Ndipo m'mayendedwe athu sitinapatuka m'njira yanu;

19 Mungakhale munatityola mokhala zirombo, Ndi kutiphimba nao mthunzi wa imfa.

20 Tikadaiwala dzina la Mulungu wathu, Ndi kutambasulira manja athu kwa mulungu wacilendo;

21 Mulungu sakadasanthula ici kodi? Pakuti adziwa zinsinsi za mtima.

22 Koma, cifukwa ca Inu, tiphedwa tsiku lonse; Tiyesedwa ngati nkhosa zakuzipha.

23 Galamukani, mugoneranji, Ambuye? Ukani, musatitaye citayire.

24 Mubisiranji nkhope yanu, Ndi kuiwala kuzunzika ndi kupsinjika kwathu?

25 Pakuti moyo wathu waweramira kupfumbi: Pamimba pathu pakangamira dziko lapansi.

26 Ukani, tithandizeni, Tiomboleni mwa cifundo canu.

45

1 Mtima wanga usefukira naco cinthu cokoma: Ndinena zopeka ine za mfumu: Lilime langa ndilo peni yofulumiza kulemba.

2 Inu ndinu wokongola ndithu kuposa ana a anthu; Anakutsanulirani cisomo pa milomo yanu: Cifukwa cace Mulungu anakudalitsani kosatha.

3 Dzimangireni lupanga lanu m'cuuno mwanu, wamphamvu inu, Ndi ulemerero wanu ndi ukulu wanu.

4 Ndipo pindulani, m'ukulu wanu yendani, Kaamba ka coonadi ndi cifatso ndi cilungamo: Ndipo dzanja lanu lidzakuphunzitsani zoopsa.

5 Mibvi yanu njakuthwa; Mitundu ya anthu igwa pansi pa Inu: Iwalasa mumtima adani a mfumu.

6 Mpando wacifumu wanu, Mulungu, ukhala nthawi zonse zamkamuyaya: Ndodo yacifumu ya ufumu wanu ndiyo ndodo yolunjika.

7 Mukonda cilungamo, ndipo mudana naco coipa: Cifukwa cace Mulungu, ndiye Mulungu wanu, wadzoza inu Ndi mafuta a cikondwerero kuposa anzanu.

8 Zobvala zanu zonse nza mure, ndi khonje, ndi kasya; M'zinyumba za mfumu zomanga ndi minyanga ya njobvu mwatoruka zoyimba za zingwe zokukondweretsani.

9 Mwa omveka anu muli ana akazi amafumu: Ku dzanja lamanja lanu aima mkazi wa mfumu wobvala golidi wa ku Ofiri.

10 Tamvera, mwana wamkaziwe, taona, tachera khutu lako; Uiwalenso mtundu wako ndi nyumba ya atate wako;

11 Potero mfumuyo adzakhumba kukoma kwako: Pakuti ndiye mbuye wako; ndipo iwe umgwadire iye.

12 Ndipo mwana wamkazi wa Turo adzafika nayo mphatso; Acuma a mwa anthu adzapempha kudziwika nanu.

13 Mwana wamkazi wa mfumu ngwa ulemerero wonse m'kati mwa nyumba: Zobvala zace nza made agolidi.

14 Adzamtsogolera kwa mfumu wabvala zamawanga-mawanga: Anamwali anzace omtsata adzafika nao kwa inu.

15 Adzawatsogolera ndi cimwemwe ndi kusekerera: Adzalowa m'nyumba ya mfumu.

16 M'malo mwa makolo ako mudzakhala ana ako, Udzawaika akhale mafumu m'dziko lonse lapansi.

17 Ndidzawakumbutsa dzina lanu m'mibadwo mibadwo: Cifukwa cace mitundu ya anthu idzayamika Inu ku nthawi za nthawi.

46

1 Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, Thandizo lopezekeratu m'masautso.

2 Cifukwa cace sitidzacita mantha, lingakhale lisandulika dziko lapansi, Angakhale mapiri asunthika, nakhala m'kati mwa nyanja;

3 Cinkana madzi ace akokoma, nacita thobvu, Nagwedezeka mapiri ndi kudzala kwace.

4 Pali mtsinje, ngalande zace zidzakondweretsa mudzi wa Mulungu. Malo oyera okhalamo Wam'mwambamwamba,

5 Mulungu ali m'kati mwace, sudzasunthika: Mulungu adzauthandiza mbanda kuca.

6 Amitundu anapokosera; maufumu anagwedezeka: Ananena mau, dziko lapansi linasungunuka.

7 Yehova wa makamu ali ndi ife; Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu.

8 Idzani, penyani nchito za Yehova, Amene acita zopululutsa pa dziko lapansi.

9 Aletsa nkhondo ku malekezero adziko lapansi; Athyola uta, nadula nthungo; Atentha magareta ndi moto.

10 Khalani cete, ndipo dziwani kuti Ine ndine Mulungu: Ndidzabuka mwa amitundu, Ndidzabuka pa dziko lapansi.

11 Yehova wa makamu ali ndi ife, Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu,

47

1 Ombani m'manja, mitundu yonse ya anthu; Pfuulirani kwa Mulungu ndi liu la kuyimbitsa.

2 Pakuti Yehova Wam'mwambamwamba ndiye woopsa; Ndiye mfumu yaikuru pa dziko lonse lapansi.

3 Atigonjetsera anthu, Naika amitundu pansi pa mapazi athu.

4 Atisankhira colowa cathu, Cokometsetsa ca Yakobo amene anamkonda.

5 Mulungu wakwera ndi mpfuu, Yehova ndi liu la lipenga.

6 Yimbirani Mulungu, yimbirani; Yimbirani Mfumu yathu, yimbirani.

7 Pakuti Mulungu ndiye Mfumu ya dziko lonse lapansi; Yimbirani ndi cilangizo.

8 Mulungu ndiye Mfumu ya amitundu: Mulungu akhala pa mpando wacifumu wace woyera.

9 Akulu a anthu asonkhana Akhale anthu a Mulungu wa Abrahamu: Pakuti zikopa za dziko lapansi nza Mulungu; Akwezeka kwakukuru Iyeyo.

48

1 Yehova ndiye wamkulu, ayenera kulemekezekadi, M'mudzi wa Mulungu wathu, m'phiri lace loyera.

2 Phiri la Ziyoni, cikhalidwe cace ncokoma Ku mbali zace za kumpoto, Ndilo cimwemwe ca dziko lonse lapansi, Mudzi wa mfumu yaikuru.

3 Mulungu adziwika m'zinyumba zace ngati msanje.

4 Pakuti, taonani, mafumuwo anasonkhana, Anapitira pamodzi.

5 Anapenya mudziwo, ndipo pamenepo anadabwa; Anaopsedwa, nathawako.

6 Pomwepo anagwidwa nako kunthunthumira; Anamva cowawa, ngati wam'cikuta.

7 Muswa zombo za ku Tarisi ndi mphepo ya kum'mawa.

8 Monga tidamva, momwemo tidapenya M'mudzi wa Yehova wa makamu, m'mudzi wa Mulungu wathu: Mulungu adzaukhazikitsa ku nthawi yamuyaya.

9 Tidalingalira za cifundo canu, Mulungu, M'kati mwa Kacisi wanu.

10 Monga dzina lanu, Mulungu, Momwemo lemekezo lanu ku malekezero a dziko lapansi: M'dzanja lamanja lanu mudzala cilungamo.

11 Likondwere phiri la Ziyoni, Asekere ana akazi a Yuda, Cifukwa ca maweruzo anu.

12 Zungulirani Ziyoni, ndipo muuzinge; Werengani nsanja zace.

13 Penyetsetsani malinga ace, Yesetsani zinyumba zace; Kuti mukaziwerengere mibadwo ikudza m'mbuyo.

14 Pakuti Mulungu ameneyo ndiye Mulungu wathu ku nthawi za nthawi: Adzatitsogolera kufikira imfa.

49

1 Dzamveni kuno, anthu inu nonse; Cherani khutu, inu nonse amakono,

2 Awamba ndi omveka omwe, Acuma ndi aumphawi omwe.

3 Pakamwa panga padzanena zanzeru; Ndipo cilingiriro ca mtima wanga cidzakhala ca cidziwitso.

4 Ndidzachera khutu kufanizo: Ndidzafotokozera cophiphiritsa canga poyimbira.

5 Ndidzaoperanji masiku oipa, Pondizinga amphulupulu onditsata kucidendene?

6 Iwo akutama kulemera kwao; Nadzitamandira pa kucuruka kwa cuma cao;

7 Kuombola mbale sangadzamuombole, Kapena kumperekera dipo kwa Mulungu:

8 (Popeza ciombolo ca moyo wao nca mtengo wace wapatali, Ndipo cilekeke nthawi zonse)

9 Kuti akhale ndi moyo osafa, Osaona cibvundi.

10 Pakuti aona anzeru amafa, Monga aonongekera wopusa, wodyerera momwemo, Nasiyira ena cuma cao.

11 Mumtima mwao ayesa kuti nyumba zao zikhala cikhalire, Ndi mokhala iwo ku mibadwo mibadwo; Achapo dzina lao padziko pao.

12 Koma munthu wa ulemu wace sakhalitsa: Afanana ndi nyama za kuthengo, afanana nazo.

13 Njira yao yino ndiyo kupusa kwao: Koma akudza m'mbuyo abvomereza mau ao.

14 Aikidwa m'manda ngati nkhosa; Mbusa wao ndi imfa: Ndipo m'mawa mwace oongoka mtima adzakhala mafumu ao; Ndipo maonekedwe ao adzanyekera kumanda, kuti pokhala pace padzasowa.

15 Koma Mulungu adzaombola moyo wanga ku mphamvu ya manda: Pakuti adzandilandira ine.

16 Usaope polemezedwa munthu, Pocuruka ulemu wa nyumba yace;

17 Pakuti pomwalira iye sadzamuka nako kanthu kali konse; Ulemu wace sutsika naye kumtsata m'mbuyo.

18 Angakhale anadalitsa moyo wace pokhala ndi moyo, Ndipo anthu akulemekeza iwe, podzicitira wekha zokoma,

19 Adzamuka ku mbadwo wa makolo ace; Sadzaona kuunika nthawi zonse.

20 Munthu waulemu, koma wosadziwitsa, Afanana ndi nyama za kuthengo, afanana nazo.

50

1 Mulungu wa milungu, Yehova, wanena, Aitana dziko lapansi kuyambira kuturuka kwa dzuwa kufikira kulowa kwace.

2 Mulungu awalira m'Ziyoni, mokongola mwangwiro.

3 Adzafika Mulungu wathu, ndipo sadzakhala cete: Moto udzanyeka pankhope pace, Ndipo pozungulira pace padzasokosera kwakukuru.

4 Kumwamba adzaitana zakumwamba, Ndi dziko lapansi, kuti aweruze anthu ace:

5 Mundisonkhanitsire okondedwa anga; Amene anapangana ndi Ine ndi nsembe.

6 Ndipo zakumwamba zionetsera cilungamo cace; Pakuti Mulungu mwini wace ndiye woweruza.

7 Imvani, anthu anga, ndipo ndidzanena; Israyeli, ndipo ndidzacita mboni pa iwe: Ine Mulungu, ndine Mulungu wako.

8 Sindikudzudzula iwe cifukwa ca nsembe zako; Popeza nsembe zako zopsereza ziri pamaso panga cikhalire.

9 Sindidzatenga ng'ombe m'nyumbamwako, Kapena mbuzi m'makola mwako.

10 Pakuti zamoyo zonse za kuthengo ndi zanga, Ndi ng'ombe za pa mapiri zikwi.

11 Ndidziwa mbalame zonse za m'mapiri: Ndipo nyama za kuthengo ziri ndi Ine.

12 Ndikamva njala, sindidzakuuza: Pakuti dziko lonse ndi langa, ndi kudzala kwace komwe.

13 Kodi ndidzadya nyama ya ng'ombe, Kapena kumwa mwazi wa mbuzi?

14 Pereka kwa Mulungu nsembe yaciyamiko; Numcitire Wam'mwambamwamba cowinda cako:

15 Ndipo undiitane tsiku la cisautso: Ndidzakulanditsa, ndipo iwe udzandilemekeza.

16 Koma kwa woipa Mulungu anena, Uli nao ciani malemba anga kulalikira, Ndi kuchula pangano langa pakamwa pako?

17 Popeza udana naco cilangizo, Nufulatira mau anga.

18 Pakuona mbala, ubvomerezana nayo, Nucita nao acigololo.

19 Pakamwa pako mpocita zocimwa, Ndipo lilime lako likonza cinyengo.

20 Ukhala, nuneneza mbale wako; Usinjirira mwana wa mai wako.

21 Izi unazicita iwe, ndipo ndinakhala cete Ine; Unayesa kuti ndifanana nawe: Ndidzakudzudzula, ndi kucilongosola pamaso pako.

22 Dziwitsani ici inu oiwala Mulungu, Kuti ndingakumwetuleni, ndipo mungasowepo mpulumutsi:

23 Wopereka nsembe yaciyamiko andilemekeza Ine; Ndipo kwa iye wosunga mayendedwe ace Ndidzamuonetsa cipulumutso ca Mulungu.

51

1 Mundicitire ine cifundo, Mulungu, Monga mwa kukoma mtima kwanu; Monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanu Mufafanize macimo anga.

2 Mubwereze kunditsuka mphulupulu yanga, Ndipo mundiyeretse kundicotsera coipa canga,

3 Cifukwa ndazindikira macimo anga; Ndipo coipa canga ciri pamaso panga cikhalire:

4 Pa Inu, Inu nokha, ndinacimwa, Ndipo ndinacicita coipaco pamaso panu: Kuti mukhale wolungama pakulankhula Inu, Mukhalenso woyera pa kuweruza kwanu.

5 Onani, ndinabadwa m'mphulupulu: Ndipo mai wanga anandilandira m'zoipa.

6 Onani, Inu mukondwera ndi zoonadi m'malo a m'katimo; Ndipo m'malo a m'tseri mudzandidziwitsa nzeru.

7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera; Munditsuke ndipo ndidzakhala wa mbu woposa matalala.

8 Mundimvetse cimwemwe ndi kusekera: Kuti mafupawo munawatyola akondwere.

9 Muzibisire nkhope yanu zolakwa zanga, Ndipo mufafanize mphulupulu zanga zonse.

10 Mundilengere mtima woyera, Mulungu; Mukonze mzimu wokhazikika m'kati mwanga.

11 Musanditaye kundicotsa pamaso panu; Musandicotsere Mzimu wanu Woyera.

12 Mundibwezere cimwemwe ca cipulumutso canu; Ndipo mzimu wakulola undigwirizize.

13 Pomwepo ndidzalangiza ocimwa njira zanu; Ndipo olakwa adzabwera kwa Inu.

14 Mundilanditse ku mlandu wa mwazi, Mulungu, Ndinu Mulungu wa cipulumutso canga; Lilime langalidzakweza Nyimbo ya cilungamo canu.

15 Ambuye, tsegulani pa milomo yanga; Ndipo pakamwa panga padzalalikira ulemekezo wanu.

16 Pakuti simukondwera ndi nsembe, mwenzi nditapereka; Nsembe yopsereza simuikonda.

17 Nsembe za Mulungu ndizo mzimu wosweka; Inu, Mulungu, simudzaupeputsa mtima wosweka ndi wolapa.

18 Citirani Ziyoni cokoma monga mwa kukondwera kwanu; Mumange malinga a miyala a Yerusalemu.

19 Pamenepo mudzakondwera nazo nsembe zacilungamo, Ndi nsembe yopsereza ndi yopsereza yathunthu: Pamenepo adzapereka Ng'ombe pa guwa lanu la nsembe.

52

1 Udzitamandiranji ndi coipa, ciphonaiwe? Cifundo ca Mulungu cikhala tsiku lonse.

2 Lilime lako likupanga zoipa; Likunga lumo lakuthwa, lakucita monyenga.

3 Ukonda coipa koposa cokoma; Ndi bodza koposa kunena cilungamo.

4 Ukonda mau onse akuononga, Lilime lacinyengo, iwe.

5 Potero Mulungu adzakupasula ku nthawi zonse, Adzakucotsa nadzakukwatula m'hema mwako, Nadzakuzula, kukucotsa m'dziko la amoyo.

6 Ndipo olungama adzaciona, nadzaopa, Nadzamseka, ndi kuti,

7 Tapenyani, suyu munthuyu amene sanamuyesa Mulungu mphamvu yace; Amene anatama kucuruka kwa cuma cace, Nadzilimbitsa m'kuipsa kwace.

8 Koma ine ndine ngati mtengo wauwisi waazitona m'nyumba ya Mulungu: Ndikhulupirira cifundo ca Mulungu ku nthawi za nthawi.

9 Ndidzakuyamikani kosatha, popeza Inu munacicita ici: Ndipo ndidzayembekeza dzina lanu, pakuti ici ncokoma, pamaso pa okondedwa anu,

53

1 Citsiru cimati mumtima mwace, Kulibe Mulungu. Acita zobvunda, acita cosalungama conyansa; Kulibe wakucita bwino.

2 Mulungu m'mwamba anaweramira pa ana a anthu, Kuti aone ngati aliko wanzeru, Wakufuna Mulungu.

3 Onse anabwerera; anabvunda mtima pamodzi; Palibe mmodzi wakucita bwino, nnena mmodzi.

4 Kodi ocita zopanda pace sadziwa? Pomadya anthu anga monga akudya mkate; Ndipo saitana Mulungu.

5 Pamenepo anaopa kwakukuru, popanda cifukwa ca kuopa: Pakuti Mulungu anamwaza mafupa a iwo akuzinga iwe; Unawacititsa manyazi, pakuti Mulungu anawakaniza.

6 Ha, cipulumutso ca Israyeli cicokere m'Ziyoni! Pakubweretsa Mulungu anthu ace a m'ndende, Yakobo adzakondwera, Israyeli adzasekera.

54

1 Ndipulumutseni, Mulungu, mwa dzina lanu, Ndipo mundiweruze ndi mphamvuyanu.

2 Imvani pemphero langa, Mulungu; Cherani khutu mau a pakamwa panga.

3 Pakuti alendo andiukira, Ndipo oopsa afunafuna moyo wanga; Sadziikira Mulungu pamaso pao.

4 Taonani, Mulungu ndiye mthandizi wanga: Ambuye ndiye wacirikiza moyo wanga.

5 Adzabwezera coipa adani anga: Aduleni m'coonadi canu.

6 Ine mwini ndidzapereka nsembe kwa Inu: Ndidzayamika dzina lanu, Yehova, pakuti nlokoma.

7 Pakuti anandilanditsa m'nsautso yonse; Ndipo ndapenya ndi diso langa ico ndakhumbira pa adani anga,

55

1 Cherani khutu pemphero langa, Mulungu; Ndipo musadzibisa pa kupemba kwanga.

2 Mveram, ndipo mundiyankhe: Ndiliralira m'kudandaula kwanga ndi kubuula;

3 Cifukwa ca mau a mdani, Cifukwa ca kundipsinja woipa; Pakuti andisenza zopanda pace, Ndipo adana nane mumkwiyo.

4 Mtima wanga uwawa m'kati mwanga; Ndipo zoopsa za imfa zandigwera.

5 Mantha ndi kunjenjemera zandidzera, Ndipo zoopsetsa zandikuta.

6 Ndipo ndinati, Ha, wina akadandipatsa mapiko onga a njiwa Mwenzi nditauluka, ndi kukhaliratu.

7 Onani, ndikadathawira kutari, Ndikadagona m'cipululu.

8 Ndikadafulumira ndipulumuke Ku mphepo yolimba ndi namondwe.

9 Aonongeni, Ambuye, gawani lilime lao: Pakuti ndaona ciwawa ndi ndeu m'mudzimo.

10 Izizo ziuzungulira pa malinga ace usana ndi usiku; Ndipo m'kati mwace muli zapanda pace ndi cobvuta.

11 M'kati mwace muli kusakaza: Ciwawa ndi cinyengo sizicoka m'makwalala ace.

12 Pakuti si mdani amene ananditonzayo; Pakadatero ndikadacilola: Amene anadzikuza pa ine sindiye munthu wondida; Pakadatero ndikadambisalira:

13 Koma ameneyo ndiwe, munthu woyenerana nane, Tsamwali wanga, wodziwana nane.

14 Tinapangirana upo wokoma, Tinaperekeza khamu la anthu popita ku nyumba ya Mulungu.

15 Imfa iwagwere modzidzimutsa, Atsikire kumanda ali amoyo: Pakuti m'mokhala mwao muli zoipa pakati pao,

16 Koma ine ndidzapfuulira kwa Mulungu; Ndipo Yehova atizandipulumutsa.

17 Madzulo, m'mawa, ndi msana ndidzadandaula, ndi kubuula, Ndipo adzamva mau anga.

18 Anaombola moyo wanga ku nkhondo yondilaka, ndikhale mumtendere: Pakuti ndiwo ambiri okangana nane.

19 Mulungu adzamva, nadzawasautsa, Ndiye wokhalabe ciyambire kale lomwe. Popeza iwowa sasinthika konse, Ndipo saopa Mulungu.

20 Anaturutsa manja ace awagwire iwo akuyanjana naye: Anaipsa pangano lace.

21 Pakamwa pace mposalala ngati mafuta amkaka, Koma mumtima mwace munali nkhondo: Mau ace ngofewa ngati mafuta oyenga, Koma anali malupanga osololasolola.

22 Umsenze Yehova nkhawa zako, ndipo Iyeadzakugwiriziza: Nthawi zonse sadzalola wolungama agwedezeke.

23 Koma Inu, Mulungu, mudzawatsitsira ku dzenje la cionongeko: Anthu okhetsa mwazi ndi acinyengo masiku ao sadzafikira nusu; Koma ine ndidzakhulupirira Inu.

56

1 Mundicitire cifundo, Mulungu, pakuti anthu afuna kundimeza: Andipsinja pondithira nkhondo tsiku lonse.

2 Adani anga afuna kundimeza tsiku lonse: Pakuti ambiri andithira nkhondo modzikuza.

3 Tsiku lakuopa ine, Ndidzakhulupirira Inu.

4 Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ace: Ndakhulupirira Mulungu, sindidzaopa; Anthu adzandicitanji?

5 Tsiku lonse atenderuza mau anga: Zolingirira zao zonse ziri pa ine kundicitira coipa.

6 Amemezana, alalira, Achereza mapazi anga, Popeza alindira moyo wanga.

7 Kodi adzapulumuka ndi zopanda pace? Gwetsani anthu mumkwiyo, Mulungu.

8 Muwerenga kuthawathawa kwanga: Sungani misozi yanga m'nsupa yanu; Kodi siikhala m'buku mwanu?

9 Pamenepo adani anga adzabwerera m'mbuyo tsiku lakuitana ine: Ici ndidziwa, kuti Mulungu abvomerezana nane.

10 Mwa Mulungu ndidzalemekeza mau ace: Mwa Yehova ndidzalemekeza mau ace.

11 Pa Mulungu ndakhulupirira, sindidzaopa; Munthu adzandicitanji?

12 Zowindira Inu Mulungu, ziri pa ine: Ndidzakucitirani zoyamika.

13 Pakuti mwalanditsa moyo wanga kuimfa: Simunatero nao mapazi anga kuti ndingagwe? Kuti ndiyende pamaso pa Mulungu M'kuunika kwa amoyo.

57

1 Mundicitire cifundo, Mulungu, mundicitire cifundo; Pakuti moyo wanga ukhulupirira Inu: Ndipo ndithawira ku mthunzi wa mapiko anu, Kufikira zosakazazo zidzapita.

2 Ndidzapfuulira kwa Mulungu Wam'mwambamwamba; Ndiye Mulungu wonditsirizira zonse.

3 Adzanditumizira m'mwamba, nadzandipulumutsa Ponditonza wofuna kundimeza; Mulungu adzatumiza cifundo cace ndi coonadi cace.

4 Moyo wanga uli pakati pa mikango; Ndigona pakati pa oyaka moto, Ndiwo ana a anthu amene mano ao ali nthungo ndi mibvi, Ndipo lilime lao ndilio lupanga lakuthwa.

5 Mukwezeke m'mwambamwa mba, Mulungu; Ulemerero wanu ukhale pamwamba pa dziko lonse lapansi.

6 Anandichera ukonde apo ndiyenda; Moyo wanga wawerama: Anandikumbira mbuna patsogolo panga; Anagwa m'kati mwace iwo okha.

7 Mtima wanga wakhazikika, Mulungu, ndakhazika mtima; Ndidzayimba, inde, ndidzayimba zolemekeza.

8 Galamuka, ulemu wanga; galamukani cisakasa ndi zeze: Ndidzauka ndekha mamawa.

9 Ndidzakuyamikirani mwa anthu, Ambuye: Ndidzakuyimbirani mwa mitundu.

10 Pakuti cifundo canu ncacikuru kufikira m'mwamba, Ndi coonadi canu kufikira mitambo.

11 Kwezekani m'mwambamwamba, Mulungu; Ulemerero wanu ukhale pamwamba m'dziko lonse lapansi.

58

1 Kodi muli cete ndithu poyenera inu kunena zolungama? Muweruza ana a anthu molunjika kodi?

2 Inde, mumtima mucita zosalungama; Pa dziko lapansi mugawira anthu ciwawa ca m'manja mwanu.

3 Oipa acita cilendo cibadwire: Asokera kuyambira kubadwa kwao, nanena bodza.

4 Ululu wao ukunga wa njoka; Akunga mphiri yogontha m'khutu, itseka m'khutu mwace.

5 Imene simvera liu la oitana, Akucita matsenga mocenieratu,

6 Tyolani mano ao m'kamwa mwao, Mulungu: Zulani zitsakano za misona ya mkango, Yehova.

7 Apitetu ngati madzi oyenda; Popiringidza mibvi yace ikhale yodukaduka.

8 Apite ngati nkhono yosungunuka; Asaone dzuwa monga mtayo,

9 Miphika yanu isanagwire moto waminga, Adzaiuluza, yaiwisi ndi yoyaka.

10 Wolungama adzakondwera pakuona kubwezera cilango: Adzasamba mapazi ace m'mwazi wa woipa.

11 Ndipo anthu adzati, Indedi, pali mphotho kwa wolungama; Indedi, pali Mulungu wakuweruza pa dziko lapansi.

59

1 Ndilanditseni kwa adani anga, Mulungu wanga: Ndiikeni pamsanje kwa iwo akundiukira.

2 Mundilanditse kwa ocita zopanda pace, Ndipo ndipulumutseni kwa anthu olira mwazi.

3 Pakuti onani, alalira moyo wanga; Amphamvu andipangira ciwembu: Osacimwa, osalakwa ine, Yehova,

4 Osawapatsa cifukwa ine, athamanga nadzikonza; Galamukani kukomana nane, ndipo penyani.

5 Ndinu Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Israyeli, Ukani kukazonda amitundu onse: Musacitire cifundo mmodzi yense wakucita zopanda pace monyenga.

6 Abwera madzulo, auwa ngati garu, Nazungulira mudzi.

7 Onani abwetuka pakamwa pao; M'milomo mwao muli lupanga, Pakuti amati, Amva ndani?

8 Koma Inu, Yehova, mudzawaseka; Mudzalalatira amitundu onse.

9 Inu, mphamvu yanga, ndidzakulindirani; Pakuti Mulungu ndiye msanje wanga.

10 Mulungu wa cifundo canga adzandikumika: Adzandionetsa tsoka la adani anga.

11 Musawapheretu, angaiwale anthu anga: Muwabalalitse mwa mphamvu yanu, ndipo muwagwetse, Ambuye, ndinu cikopa cathu.

12 Pakamwa pao acimwa ndi mau onse a pa milomo yao, Potero akodwe m'kudzitamandira kwao, Ndiponso cifukwa ca kutemberera ndi bodza azilankhula.

13 Muwathe mumkwiyo, muwagurule psiti: Ndipo adziwe kuti Mulungu ndiye woweruza m'Yakobo, Kufikira malekezero a dziko la pansi.

14 Ndipo abwere madzulo, auwe ngati garu, Nazungulire mudzi.

15 Ayendeyende ndi kufuna cakudya, Nacezere osakhuta.

16 Koma ine, ndidzayimbira mphamvu yanu; Inde ndidzayimbitsa cifundo canu mamawa: Pakuti Inu mwakhala msanje wanga, Ndi pothawirapo ine tsiku la nsautso yanga.

17 Ndidzayimbira zakukulemekezani Inu, mphamvu yanga: Pakuti Mulungu ndiye msanje wanga, Mulungu wa cifundo canga.

60

1 Mwatitaya Mulungu, mwatipasula; Mwakwiya; tibwezereni.

2 Mwagwedeza dziko, mwaling'amba: Konzani ming'alu yace; pakuti ligwedezeka.

3 Mwaonetsa anthu anu zowawa: Mwatimwetsa vinyo wotinjenjemeretsa.

4 Koma mwapatsa mbendera akuopa Inu, Aikweze cifukwa ca coonadi.

5 Kuti okondedwa anu alanditsidwe, Pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja, ndipo mutibvomereze.

6 Mulungu walankhula m'ciyero cace; ndidzakondwerera: Ndidzagawa Sekemu, ndidzayesa muyeso cigwa ca Sukoti.

7 Gileadi ndi wanga, Manasenso ndi wanga; Ndipo Efraimu ndi mphamvu ya mutu wanga; Yuda ndiye wolamulira wanga,

8 Moabu ndiye mkhate wanga; Pa Edomu ndidzaponya nsapato yanga: Filistiya, pfuulatu cifukwa ca ine.

9 Adzandifikitsa ndani m'mudzi wa m'linga? Adzanditsogolera ndani ku Edomu?

10 Si ndinu, Mulungu, amene mwantaya? Osaturuka nao makamu athu, Mulungu.

11 Tithandizeni kunsautso; Kuti cipulumutso ca munthu ndi cabe.

12 Mwa Mulungu tidzacita molimbika mtima, Ndipo Iye adzapondereza otisautsa.

61

1 Imvani mpfuu wanga, Mulungu; Mverani pemphero langa.

2 Ku malekezero a dziko lapansi ndidzapfuulira kwa Inu, pomizika mtima wanga: Nditsogolereni ku thanthwe londiposa ine m'kutalika kwace.

3 Pakuti munakhala pothawirapo panga; nsanja yolimba pathawa mdani ine.

4 Ndidzagonera-gonerabe m'cihemamwanu; Ndidzathawira mobisalamo m'mapiko anu.

5 Pakuti Inu, Mulungu, mudamva zowinda zanga; Munandipatsa colowa ca iwo akuopa dzina lanu.

6 Mudzatalikitsa moyo wa mfumu: Zaka zace zidzafikira mibadwo mibadwo.

7 Adzakhala nthawi zonse pamaso pa Mulungu; Mumpatse cifundo ndi coonadi zimsunge.

8 Potero ndidzayimba zolemekeza dzina lanu ku nthawi zonse, Kuti ndicite zowinda zanga tsiku ndi tsiku.

62

1 Moyo wanga ukhalira cete Mulungu yekha: Cipulumutso canga cifuma kwa Iye.

2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi cipulumutso canga; Msanje wanga, sindidzagwedezeka kwakukuru.

3 Mudzambvumbvulukira munthu mpaka liti, Kumupha iye, nonsenu, Monga khoma lopendekeka, ndi mpanda woweyeseka?

4 Komatu amkhaliraupo kuti amkankhire pansi ulemu wace; Akondwera nao mabodza; Adalitsa ndi m'kamwa mwao, Koma atemberera mumtima.

5 Moyo wanga, ukhalire cete Mulungu yekha; Pakuti ciyembekezo canga cifuma kwa Iye,

6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi cipulumutso canga, Msanje wanga, sindidzagwedezeka.

7 Pa Mulungu pali cipulumutso canga ndi ulemerero wanga: Thanthwe la mphamvu yanga ndi pothawirapo panga mpa Mulungu.

8 Khulupirani pa Iye nyengo zonse, anthu inu: Tsanulirani mitima yanu pamaso pace: Mulungu ndiye pothawirapo ife.

9 Indetu, anthu acabe ndi mpweya, ndipo anthu akuru ndi bodza: Pakuwayesa apepuka; Onse pamodzi apepuka koposa mpweya,

10 Musakhulupirire kusautsa, ndipo musatama cifwamba; Cikacuruka cuma musakhazikepo mitima yanu.

11 Mulungu ananena kamodzi, ndinacimva kawiri: Kuti mphamvu ndi yace ya Mulungu:

12 Cifundonso ndi canu, Ambuye: Cifukwa Inu musudzula munthu ali yense monga mwa nchito yace.

63

1 Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga; ndidzakufunani m'matanda kuca: Moyo wanga ukumva ludzu la kwa Inu, thupi langa lilirira Inu, M'dziko louma ndi lotopetsa, lopanda madzi.

2 Kuti ndione mphamvu yanu ndi ulemerero wanu, Monga ndinakuonani m'malo oyera.

3 Pakuti cifundo canu ciposa moyo makomedwe ace; Milomo yanga idzakulemekezani.

4 Potero ndidzakuyamikani m'moyo mwanga; Ndidzakweza manja anga m'dzina lanu.

5 Mudzakhutitsa moyo wanga ngati ndi mafuta ndi zonona; Ndipo pakamwa panga ndidzakulemekezani ndi milomo yakupfuula mokondwera;

6 Pokumbukira Inu pa kama wanga, Ndi kulingalira za Inu maulonda a usiku.

7 Pakuti munakhala mthandizi wanga; Ndipo ndidzapfuula mokondwera mu mthunzi wa mapiko anu.

8 Moyo wanga uumirira Inu: Dzanja lamanja lanu lindigwiriziza.

9 Koma iwo amene afuna moyo wanga kuti auononge, Adzalowa m'munsi mwace mwa dziko.

10 Adzawapereka ku mphamvu ya lupanga; Iwo adzakhala gawo la ankhandwe.

11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu; Yense wakulumbirira iye adzatamandira; Pakuti pakamwa pa iwo onena bodza padzatsekedwa.

64

1 Imvani Yehova, mau anga, m'kudandaula kwanga; Sungani moyo wanga angandiopse mdani.

2 Ndibiseni pa upo wacinsinsi wa ocita zoipa; Pa phokoso la ocita zopanda pace:

3 Amene anola lilime lao ngati lupanga, Napiringidza mibvi yao, ndiyo mau akuwawitsa;

4 Kuponyera wangwiro mobisika: Amponyera modzidzimutsa, osaopa.

5 Alimbikitsana m'cinthu coipa; Apangana za kuchera misampha mobisika; Akuti, Adzaiona ndani?

6 Afunafuna zosalungama; kusanthula, asanthuladi kutha; Cingakhale ca m'kati mwace mwa munthu, ndi mtima wozama.

7 Koma Mulungu adzawaponyera mubvi; Adzalaswa modzidzimutsa,

8 Adzawakhumudwitsa, lilime lao lidzawatsutsa; Onse akuwaona adzawathawa.

9 Ndipo anthu onse adzacita mantha; Nadzabukitsa cocita Mulungu, Nadzasamalira nchito yace.

10 Wolungama adzakondwera mwa Yehova, nadzakhulupirira Iye; Ndipo oongoka mtima onse adzalemekeza.

65

1 M'Ziyoni akulemekezani Inu mwacete, Mulungu: Adzakucitirani Inu cowindaci.

2 Wakumva pemphero Inu, Zamoyo zonse zidzadza kwa Inu.

3 Mphulupulu zinandilaka; Koma mudzafafaniza zolakwa zathu.

4 Wodala munthuyo mumsankha, ndi kumyandikizitsa, Akhale m'mabwalo anu: Tidzakhuta nazo zokoma za m'nyumba yanu, Za m'malo oyera a Kacisi wanu.

5 Mudzatiyankha nazo zoopsa m'cilungamo, Mulungu wa cipulumutso cathu; Ndinu cikhulupiriko ca malekezero Onse a dziko lapansi, Ndi ca iwo okhala kutali kunyanja:

6 Ndinu amene mukhazikitsa mapiri ndi mphamvu yanu; Pozingidwa naco cilimbiko.

7 Amene atontholetsa kukuntha kwa nyanja, kukuntha kwa mafunde ace, Ndi phokoso la mitundu ya anthu.

8 Ndipo iwo akukhala kumalekezero adzacita mantha cifukwa ca zizindikilo zanu; Mukondweretsa apo paturukira dzuwa, ndi apo lilowera.

9 Muceza nalo dziko lapansi, muhthirira, Mulilemeza kwambiri; Mtsinje wa Mulungu udzala nao madzi: Muwameretsera tirigu m'mene munakonzera nthaka.

10 Mukhutitsa nthaka yace yolima; Mufafaniza nthumbira zace? Muiolowetsa ndi mbvumbi; Mudalitsa mmera wace.

11 Mubveka cakaci ndi ukoma wanu; Ndipo mabande anu akukha zakuca.

12 Akukha pa mabusa a m'cipululu; Ndipo mapiri azingika naco cimwemwe.

13 Podyetsa mpodzaza ndi zoweta; Ndipo zigwa zakutidwa ndi tirigu; Zipfuula mokondwera, inde ziyimbira.

66

1 Pfuulirani kwa Mulungu, dziko lonse lapansi.

2 Yimbirani ulemerero wa dzina lace; Pomlemekeza mumcitire ulemerero.

3 Nenani kwa Mulungu, Ha, nchito zanu nzoopsa nanga! Cifukwa ca mphamvu yanu yaikuru adani anu adzagonjera Inu,

4 Dziko lonse lapansi lidzakugwadirani, Ndipo lidzakuyimbirani; Adzayimbira dzina lanu.

5 Idzani, muone nchito za Mulungu; Zocitira Iye ana a anthu nzoopsa.

6 Anasanduliza nyanja ikhale mtunda: Anaoloka mtsinje coponda pansi: Apo tinakondwera mwa Iye.

7 Acita ufumu mwa mphamvu yace kosatha; Maso ace ayang'anira amitundu; Opikisana ndi Iye asadzikuze.

8 Lemekezani Mulungu wathu, mitundu ya anthu inu, Ndipo mumveketse liu la cilemekezo cace:

9 Iye amene asunga moyo wathu tingafe, Osalola phazi lathu literereke.

10 Pakati munatiyesera, Mulungu: Munatiyenga monga ayenga siliya.

11 Munapita nafe kuukonde; Munatisenza cothodwetsa pamsana pathu.

12 Munapititsa anthu oberekeka pamwamba pamitu pathu; Tinapyola moto ndi madzi; Koma munatifikitsa potitsitsimutsa.

13 Ndidzalowa m'nyumba yanu ndi nsembe zopsereza, Ndidzakucitirani zowinda zanga,

14 Zimene inazichula milomo yanga, Ndinazinena pakamwa panga pasautsika ine.

15 Ndidzakufukizirani nsembe zapsereza zonona, Pamodzi ndi cofukiza ca mphongo za nkhosa; Ndidzakonza ng'ombe pamodzi ndi mbuzi.

16 Idzani, imvani, inu nonse akuopa Mulungu, Ndipo ndidzafotokozera zonse anazicitira moyo wanga,

17 Ndinampfuulira Iye pakamwa panga, Ndipo ndinamkuza ndi lilime langa,

18 Ndikadasekera zopanda pace m'mtima mwanga, Ambuye sakadamvera:

19 Koma Mulungu anamvadi; Anamvera mau a pemphero langa,

20 Wolemekezeka Mulungu, Amene sanandipatutsira ine pemphero langa, kapena cifundo cace.

67

1 Aticitire cifundo Mulungu, ndi kutidalitsa, Atiwalitsire nkhope yace;

2 Kuti njira yanu idziwike pa dziko lapansi, Cipulumutso canu mwa amitundu onse.

3 Anthu akuyamikeni, Mulungu; Anthu onse akuyamikeni.

4 Anthu akondwere, napfuule makondwera; Pakuti mudzaweruza anthu malunjika, Ndipo mudzalangiza anthu pa dziko lapansi.

5 Anthu akuyamikeni, Mulungu; Anthu onse akuyamikeni.

6 Dziko lapansi lapereka zipatso zace: Mulungu, Mulungu wathu adzatidalitsa.

7 Mulungu adzatidalitsa; Ndipo malekezero onse a dziko lapansi adzamuopa Iye,

68

1 Auke Mulungu, abalalike adani ace; Iwonso akumuda athawe pamaso pace.

2 Muwacotse monga utsi ucotseka; Monga phula lisungunuka pamoto, Aonongeke oipa pamaso pa Mulungu.

3 Koma olungama akondwere; atumphe ndi cimwemwe pamaso pa Mulungu; Ndipo asekere naco cikondwerero.

4 Yimbirani Yehova, liyimbireni Nyimbo dzina lace; Undirani mseu Iye woberekekayo kucidikha; Dzina lace ndiye Yehova; ndipo tumphani ndi cimwemwe pamaso pace.

5 Mulungu, mokhala mwace mayera, Ndiye Atate wa ana amasiye, ndi woweruza wa akazi amasiye.

6 Mulungu amangitsira banjaanthu a pa okha; Aturutsa am'ndende alemerere; Koma opikisana naye akhala m'dziko lopanda madzi.

7 Pakuturuka paja, Inu Mulungu, ndi kutsogolera anthu anu, Pakuyenda paja Inu m'cipululu;

8 Dziko lapansi linagwedezeka, Inde thambo linakhapamaso pa Mulungu; Sinai lomwe linagwedezeka pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israyeli.

9 Inu, Mulungu, munabvumbitsa cimvula, Munatsitsimutsa colowa canu pamene cidathodwa.

10 Gulu lanu linakhala m'dziko muja: Mwa ukoma wanu munalikonzera ozunzika, Mulungu.

11 Ambuye anapatsa mau: Akazi akulalikira uthengawo ndiwo khamu lalikuru.

12 Mafumu a magulu a ankhondo athawathawa: Ndipo mkazi amene akhala kwao agawa zofunkha.

13 Pogona inu m'makola a zoweta, Mukhala ngati mapiko a njiwa okulira ndi siliva, Ndi nthenga zace zokulira ndi golidi woyenga wonyezimira.

14 Pamene Wamphamvuyonse anabalalitsa mafumu m'dzikomo, Munayera ngati matalala m'Salimoni.

15 Phiri la Basana ndilo phiri la Mulungu; Phiri la Basana ndilo phiri la mitu mitu.

16 Mucitiranji nsanje mapiri inu a mitu mitu, Ndi phirilo Mulungu analikhumba, akhaleko? Inde, Yehova adzakhalabe komweko kosatha.

17 Magareta a Mulungu ndiwo zikwi makumi awiri, inde zikwi zowirikiza-wirikiza: Ambuye ali pakati pao, monga m'Sinai, m'malo opatulika,

18 Munakwera kumka kumwamba, munapita nao undende kuuyesa ndende; Munalandira zaufulu mwa anthu, Ngakhale mwa opikisana nanu, kuti Yehova Mulungu akakhale nao.

19 Wolemekezeka Ambuye, tsiku ndi tsiku atisenzera katundu, Ndiye Mulungu wa cipulumutso cathu.

20 Mulungu akhala kwa ife Mulungu wa cipulumutso; Ndipo Yehova Ambuye ali nazo zopulumutsira kuimfa.

21 Indedi Mulungu adzaphwanya mutu wa adani ace, Pakati pa mutu pa iye woyendabe m'kutsutsika kwace.

22 Ambuye anati, Ndidzawatenganso ku Basana, Ndidzawatenganso kozama kwa nyanja:

23 Kuti ubviike phazi lako m'mwazi, Kuti malilime a agaru ako alaweko adani ako.

24 Anapenya mayendedwe anu, Mulungu, Mayendedwe a Mulungu wanga, Mfumu yanga, m'malo oyera.

25 Oyimbira anatsogolera, oyimba zoyimba anatsata m'mbuyo, Pakatipo anamwali oyimba mangaka.

26 Lemekezani Mulungu m'masonkhano, Ndiye Ambuye, inu a gwero la Israyeli.

27 Apo pali Benjamini wamng'ono, wakuwacita ufumu, Akuru a Yuda, ndi a upo wao, Akulu a Zebuloni, akulu a Naftali.

28 Mulungu wako analamulira mphamvu yako: Limbitsani, Mulungu, cimene munaticitira.

29 Cifukwa ca Kacisi wanu wa m'Yerusalemu Mafumu adzabwera naco caufulu kukupatsani.

30 Dzudzulani cirombo ca m'bango, Khamu la mphongo ndi zipfulula za anthu, Yense wakudzigonjera ndi ndarama zasiliva; Anabalalitsa mitundu ya anthu ya kukondwera nayo nkhondo.

31 Akulu adzafumira ku Aigupto; Kushi adzafulumira kutambalitsa manja ace kwa Mulungu.

32 Yimbirani Mulungu, maufumu a dziko lapansi inu; Yimbirani Ambuye zomlemekeza;

33 Kwa Iye wakuberekeka pamwambamwamba, oyambira kale lomwe; Taonani; amveketsa liu lace, ndilo liu lamphamvu.

34 Bvomerezani kuti mphamvu nja Mulungu; Ukulu wace uli pa Israyeli, Ndi mphamvu yace m'mitambo.

35 Inu Mulungu, ndinu woopsa m'malo oyera anu; Mulungu wa Israyeli ndiye amene apatsa anthu ace mphamvu ndi cilimbiko. Alemekezeke Mulungu.

69

1 Ndipulumutseni Mulungu; Pakuti madzi afikira moyo wanga.

2 Ndamira m'thope lozama, lopanda poponderapo; Ndalowa m'madzi ozama, ndipo cigumula candimiza.

3 Ndalema ndi kupfuula kwanga; kum'mero kwauma gwa: M'maso mwanga mwada poyembekeza Mulungu wanga.

4 Ondida kopanda cifukwa acuruka koposa tsitsi la pamutu panga; Ofuna kunditha, ndiwo adani anga monama, ali ndi mphamvu: Pamenepo andibwezetsa cosafunkha ine.

5 Mulungu, mudziwa kupusa kwanga; Ndipo kutsutsika kwanga sikubisikira Inu.

6 Iwo akuyembekeza Inu, Ambuve Yehova wa makamu, asacite manyazi cifukwa ca ine: Iwo ofuna Inu, Mulungu wa Israyeli, asapepulidwe cifukwa ca ine.

7 Pakuti ndalola cotonza cifukwa ca Inu: Cimpepulo cakuta nkhope yanga,

8 Abale anga andiyesa mlendo, Ndi ana a mai wanga andiyesa wa mtundu wina.

9 Pakuti cangu ca pa nyumba yanu candidya; Ndi zotonza za iwo otonza Inu zandigwera ine.

10 Ndipo ndinalira pa kusala kwa moyo wanga, Koma uku kunandikhalira cotonza.

11 Ndipo cobvala canga ndinayesa ciguduli, Koma amandiphera mwambi.

12 Okhala pacipata akamba za ine; Ndipo oledzera andiyimba.

13 Koma ine, pemphero langa liri kwa Inu, Yehova, m'nyengo yolandirika; Mulungu, mwa cifundo canu cacikuru, Mundibvomereze ndi coonadi ca cipulumutso canu.

14 Mundilanditse kuthope, ndisamiremo: Ndilanditseni kwa iwo akundida, ndi kwa madzi ozama.

15 Cigumula cisandifotsere, Ndipo cakuya cisandimize; Ndipo asanditsekere pakamwa pace pa dzenje.

16 Mundiyankhe Yehova; pakuti cifundo canu ncokoma; Munditembenukire monga mwa unyinji wa nsoni zokoma zanu.

17 Ndipo musabisire nkhope yanu mtumiki wanu; Pakuti ndisautsika ine; mundiyankhe msanga.

18 Yandikizani moyo wanga, ndi kuuombola; Ndipulumutseni cifukwa ca adani anga,

19 Mudziwa cotonza canga, ndi manyazi anga, ndi cimpepulo canga: Akundisautsa ali pamaso panu,

20 Cotonza candiswera mtima, ndipo ndidwala ine; Ndipo ndinayembekeza wina wondicitira cifundo, koma palibe; Ndinayembekeza onditonthoza mtima, osawapeza.

21 Ndipo anandipatsa ndulu ikhale cakudya canga; Nandimwetsa vinyo wosasa pomva ludzu ine.

22 Gome lao likhale msampha pamaso pao; Pokhala ndi mtendere iwo, likhale khwekhwe.

23 M'maso mwao mude, kuti asapenye; Ndipo munjenjemeretse m'cuuno mwao kosalekeza.

24 Muwatsanulire mkwiyo wanu, Ndipo moto wa ukali wanu uwagwere.

25 Pokhala pao pakhale bwinja; M'mahema mwao musakhale munthu.

26 Pakuti alondola amene Inu munampanda; Ndipo akambirana za zowawa zao za iwo amene munawalasa.

27 Onjezani mphulupulu pa mphulupulu zao; Ndipo asafikire cilungamo canu.

28 Afafanizidwe m'buku lamoyo, Ndipo asalembedwe pamodzi ndi olungama,

29 Koma ine ndine wozunzika ndi womva zowawa; Cipulumutso canu, Mulungu, cindikweze pamsanje.

30 Ndidzalemekeza dzina la Mulungu ndi kuliyimbira, Ndipo ndidzambukitsa ndi kumyamika.

31 Ndipo cidzakomera Yehova koposa ng'ombe, Inde mphongo za nyanga ndi ziboda,

32 Ofatsa anaciona, nakondwera: Ndipo inu, ofuna Mulungu, mtima wanu ukhale ndi moyo.

33 Pakuti Yehova amvera aumphawi, Ndipo sapeputsa am'ndende ace.

34 Zakumwamba ndi dziko lapansi zimlemekeze, Nyanja ndi zonse zoyenda m'mwemo;

35 Pakuti Mulungu adzapulumutsa Ziyoni, nadzamanga midzi ya Yuda; Ndipo iwo adzakhala komweko, likhale lao lao.

36 Ndipo mbumba ya atumiki ace idzalilandira; Ndipo iwo akukonda dzina lace adzakhalam'mwemo.

70

1 Fulumirani kundipulumutsa, Mulungu; Fulumirani kundithandiza, Yehova.

2 Acite manyazi, nadodome Amene afuna moyo wanga: Abwezedwe m'mbuyo, napepulidwe. Amene akonda kundicitira coipa,

3 Abwerere, kukhale mphotho ya manyazi ao Amene akuti, Hede, hede.

4 Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu; Nanene kosalekeza iwo akukonda cipulumutso canu, Abuke Mulungu.

5 Koma ine ndine wozunzika ndi waumphawi; Mundifulumirire, Mulungu: Inu ndinu mthandizi wanga ndi mpulumutsi wanga; Musacedwe, Yehova.

71

1 Ndikhulupirira Inu, Yehova: Ndisacite manyazi nthawi zonse.

2 Ndikwatuleni m'cilungamo canu, ndi kundilanditsa: Ndicherereni khutu lanu ndi kundipulumutsa.

3 Mundikhalire thanthwe lokhalamo, lopitako kosaleka; Mwalamulira kundipulumutsa; Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,

4 Ndilanditseni, Mulungu wanga, m'dzanja la woipa, M'dzanja la munthu wosalungama ndi waciwawa.

5 Pakuti Inu ndinu ciyembekezo canga, Ambuye Yehova; Mwandikhalira wokhulupirika kuyambira ubwana wanga.

6 Inu munandigwirizizakuyambira ndisanabadwe: Kuyambira pa thupi la mai wanga wondicitira zokoma ndinu; Ndidzakulemekezani kosalekeza.

7 Ndikhala codabwiza kwa ambiri; Koma Inu ndinu pothawira panga polimba.

8 M'kamwa mwanga mudzadzala lemekezo lanu, Ndi ulemu wanu tsiku lonse.

9 Musanditaye mu ukalamba wanga; Musandisiye, pakutha mphamvu yanga.

10 Pakuti adani anga alankhula za ine; Ndipo iwo akulalira moyo wanga apangana upo,

11 Ndi kuti, Wamsiya Mulungu: Mlondoleni, mgwireni; popeza palibe wompulumutsa,

12 Musandikhalire kutali, Mulungu; Fulumirani kundithandiza, Mulungu;

13 Adani a moyo wanga acite manyazi, nathawe; Cotonza ndi cimpepulo zikute ondifunira coipa,

14 Koma ine ndidzayembekeza kosaleka, Ndipo ndidzaonjeza kukulemekezani.

15 Pakamwa panga padzafotokozera cilungamo canu, Ndi cipulumutso canu tsiku lonse; Pakuti sindidziwa mawerengedwe ace.

16 Ndidzamuka mu mphamvu ya Ambuye Yehova; Ndidzachula cilungamo canu, inde canu cokha.

17 Mulungu, mwandiphunzitsa kuyambira ubwana wanga; Ndipo kufikira lero ndilalikira zodabwiza zanu.

18 Poteronso pokalamba ine ndi kukhala nazo imvi musandisiye, Mulungu; Kufikira nditalalikira mbadwo uwu za dzanja lanu, Mphamvu yanu kwa onse akudza m'mbuyo.

19 Cilungamo canunso, Mulungu, cifikira kuthambo; Inu amene munacita zazikuru, Akunga Inu ndani, Mulungu?

20 Inu, amene munationetsa nsautso zambiri ndi zoipa, Mudzatipatsanso moyo, Ndi kutitenganso munsi mwa dziko.

21 Mundionjezere ukulu wanga, Ndipo munditembenukire kundisangalatsa,

22 Ndiponso ndidzakuyamikani ndi cisakasa, Kubukitsa coonadi canu, Mulungu wanga; Ndidzakuyimbirani Nyimbo ndi zeze, Ndinu Woyerayo wa Israyeli.

23 Milomo yanga idzapfuula mokondwera poyimbira Inu Nyimbo; Inde, moyo wanga umene munaombola.

24 Lilime langa lomwe lidzalankhula za cilungamo canu tsiku lonse: Pakuti ofuna kundicitira coipa acita manyazi, nadodoma.

72

1 Patsani mfumu maweruzo anu, Mulungu, Ndi mwana wa mfumu cilungamo canu.

2 Potero adzanenera anthu anu mlandu ndi m'cilungamo, Ndi ozunzika anu ndi m'ciweruzo.

3 Mapiri adzatengera anthu mtendere, Timapiri tomwe, m'cilungamo.

4 Adzaweruza ozunzika a mwa anthu, Adzapulumutsa ana aumphawi, Nadzaphwanya wosautsa.

5 Adzakuopani momwe likhalira dzuwa ndi mwezi, Kufikira mibadwo mibadwo.

6 Adzanga mvula yakugwa pa udzu wosenga: Monga mvula yothirira dziko.

7 Masiku ace wolungama adzakhazikika; Ndi mtendere wocuruka, kufikira sipadzakhala mwezi.

8 Ndipo adzacita ufumu kucokera kunyanja kufikira kunyanja, Ndi kucokera ku Mtsinje kufikira malekezero a dziko lapansi.

9 Okhala m'cipululu adzagwadira pamaso pace; Ndi adani ace adzaluma nthaka.

10 Mafumu a ku Tarisi ndi ku Zisumbuzo adzabwera naco copereka; Mafumu a ku Sheba ndi Seba adzadza nazo mphatso,

11 Inde mafumu onse adzamgwadira iye: Amitundu onse adzamtumikira.

12 Pakuti adzapulumutsa waumphawi wopfuulayo; Ndi wozunzika amene alibe mthandizi.

13 Adzacitira nsoni wosauka ndi waumphawi, Nadzapulumutsa moyo wa aumphawi,

14 Adzaombola moyo wao ku cinyengo ndi ciwawa; Ndipo mwazi wao udzakhala wa mtengo pamaso pace:

15 Ndipo iye adzakhala ndi moyo; ndipo adzampatsa golidi wa ku Sheba; Nadzampempherera kosalekeza; Adzamlemekeza tsiku lonse.

16 M'dzikomo mudzakhala dzinthu dzocuruka pamwamba pa mapiri; Zipatso zace zidzati waa, ngati za ku Lebano: Ndipo iwo a m'mudzi adzaphuka ngati msipu wapansi.

17 Dzina lace lidzakhala kosatha: Momwe likhalira dzuwa dzina lace lidzamvekera zidzukulu: Ndipo anthu adzadalitsidwa mwa Iye; Amitundu onse adzamucha wodala.

18 Wolemekezeka Yehova Mulungu, Mulungu wa Israyeli, Amene acita zodabwiza yekhayo:

19 Ndipo dzina lace la ulemerero lidalitsike kosatha; Ndipo dziko lonse lapansi lidzale nao ulemerero wace. Amen, ndi Amen.

73

1 Indedi Mulungu acitira Israyeli zabwino, Iwo a mtima wa mbe.

2 Koma ine, ndikadagwa; Mapazi anga akadaterereka,

3 Pakuti ndinacitira nsanje odzitamandira, Pakuona mtendere wa oipa,

4 Pakuti palibe zomangira pakufa iwo: Ndi mphamvu yao niolimba,

5 Sabvutika monga anthu ena; Sasautsika monga anthu ena.

6 Cifukwa cace kudzikuza kunga unyolo pakhosi pao; Acibvala ciwawa ngati malaya.

7 Kunenepa kwao kutuzulitsa maso ao: Malingaliro a mitima yao asefukira.

8 Acita zaphwete nalankhula moipa za kusautsa: Alankhula modzitama.

9 Pakamwa pao anena zam'mwamba, Ndipo lilime lao liyendayenda m'dziko lapansi.

10 Cifukwa cace anthu ace amabwera kudza kuno: Ndipo cikho codzala ndi madzi acigugudiza.

11 Namati, Akacidziwa bwanji Mulungu? Kodi Wam'mwambamwamba ali nayonzeru?

12 Tapenyani, oipa ndi awa; Ndipo pokhazikika cikhazikikire aonjezerapo pa cuma cao.

13 Indedi, ndinayeretsa mtima wanga kwacabe, Ndipo ndinasamba m'manja mosalakwa;

14 Popeza andisautsa tsiku lonse, Nandilanga mamawa monse,

15 Ndikadati, Ndidzafotokozera cotere, Taonani, ndikadacita cosakhulupirika ndi mbadwo wa ana ako.

16 Pamene ndinayesa kudziwitsa ici, Ndinabvutika naco;

17 Mpaka ndinalowa m'zoyera za Mulungu, Ndi kulingalira citsiriziro cao.

18 Indedi muwaika poterera: Muwagwetsa kuti muwaononge.

19 Ha! m'kamphindi ayesedwa bwinja; Athedwa konse ndi zoopsya.

20 Monga anthu atauka, apepula loto; Momwemo, Inu Ambuye, pakuuka mudzapeputsa cithunzithunzi cao.

21 Pakuti mtima wanga udawawa, Ndipo ndinalaswa m'imso zanga;

22 Ndinali wam'thengo, wosadziwa kanthu; Ndinali ngati nyama pamaso panu.

23 Koma ndikhala ndi Inu cikhalire: Mwandigwira dzanja langa la manja.

24 Mudzanditsogolera ndi uphungu wanu, Ndipo mutatero, mudzandilandira m'ulemerero,

25 Ndiri ndi yani Kumwamba, koma Inu? Ndipo Pa dziko lapansi palibe wina wondikonda koma Inu.

26 Likatha thupi langa ndi mtima wanga: Mulungu ndiye thanthwe la mtima wanga, ndi colandira canga cosatha.

27 Pakuti, taonani, iwo okhala patali ndi Inu adzaonongeka; Muononga onse akupembedza kwina, kosiyana ndi Inu.

28 Koma ine, kundikomera kuyandikiza kwa Mulungu: Ndimuyesa Ambuye Yehova pathawirapo ine, Kuti ndifotokozere nchito zanu zonse,

74

1 Mulungu, munatitayiranji citayire? Mkwiyo wanu ufukiranji pa nkhosa za kubusa kwanu?

2 Kumbukilani msonkhano wanu, umene munaugula kale, Umene munauombola ukhale pfuko la colandira canu; Phiri La Ziyoni limene mukhalamo.

3 Nyamulani mapazi anu kukapenya mapasukidwe osatha, Zoipa zonse adazicita mdani m'malo opatulika.

4 Otsutsana ndi Inu abangula pakati pa msonkhano wanu; Aika mbendera zao zikhale zizindikilo.

5 Anaoneka ngati osamula nkhwangwa kunkhalango.

6 Ndipo tsopano aphwanya zosemeka zace zonse Ndi nkhwangwa ndi nyundo,

7 Anatentha malo anu opatulika; Anaipsa ndi kugwetsa pansi mokhalamo dzina lanu.

8 Ananena mumtima mwao, Tiwapasule pamodzi; Anatentha zosonkhaniramo za Mulungu zonse, m'dzikomo.

9 Sitiziona zizindikilo zathu; Palibenso mneneri; Ndipo mwa ife palibe wina wakudziwa mpaka liti.

10 Wotsutsanayo adzatonza kufikira liti, Mulungu? Kodi mdani adzanyoza dzina lanu nthawi yonse?

11 Mubwezeranji dzanja lanu, ndilo dzanja lamanja lanu? Muliturutse ku cifuwa canu ndipo muwatheretu.

12 Koma Mulungu ndiye mfumu yanga kuyambira kale, Wocita zakupulumutsa pakati pa dziko lapansi.

13 Mudagawa nyanja ndi mphamvu yanu; Mudaswa mitu ya zoopsa za m'madzi.

14 Mudaphwanya mitu ya livyatanu; Mudampereka akhale cakudya ca iwo a m'cipululu.

15 Mudagawa kasupe ndi mtsinje; Mudaphwetsa mitsinje yaikuru.

16 Usana ndi wanu, usikunso ndi wanu: Munakonza kuunika ndi dzuwa.

17 Munaika malekezero onse a dziko lapansi; Munalenga dzinja ndi malimwe.

18 Mukumbukile ici, Yehova, mdaniyo anatonza, Ndipo anthu opusa ananyoza dzina lanu.

19 Musapereke moyo wa njiwa yanu kwa cirombo; Musamaiwala moyo wa ozunzika anu nthawi yonse.

20 Samalirani cipanganoco; Pakuti malo amdima a m'dziko adzala ndi zokhalamo ciwawa.

21 Okhalira mphanthi asabwere nao manyazi; Wozunzika ndi waumphawi alemekeze dzina lanu.

22 Nyamukani, Mulungu, mudzinenere mlandu nokha; Kumbukilani momwe akutonzani wopusa tsiku lonse.

23 Musaiwale mau a iwo otsutsana ndi Inu; Kusokosera kwa iwo akuukirani Inu kumakweca kosaleka.

75

1 Tikuyamikani Inu, Mulungu; Tiyamika, pakuti dzina lanu liri pafupi; Afotokozera zodabwiza zanu,

2 Pakuona nyengo yace ndidzaweruza molunjika.

3 Lasungunuka dziko lapansi, ndi onse okhalamo; Ndinacirika mizati yace.

4 Ndinati kwa odzitamandira, Musamacita zodzitamandira; Ndi kwa oipa, Musamakweza nyanga;

5 Musamakwezetsa nyanga yanu; Musamalankhula ndi khosi louma.

6 Pakuti kukuzaku sikucokera kum'mawa, Kapena kumadzulo, kapena kucipululu,

7 Pakuti Mulungu ndiye woweruza; Acepsa wina, nakuza wina.

8 Pakuti m'dzanja la Yehova muli cikho; Ndi vinyo wace acita thobvu; Cidzala ndi zosanganizira, ndipo atsanulako: Indedi, oipa onse a pa dziko lapansi adzamwa Nadzagugudiza nsenga zace.

9 Koma ine ndidzalalikira kosalekeza, Ndidzayimbira zomlemekeza Mulungu wa Yakobo.

10 Ndipo ndidzatseteka nyanga zonse za oipa; Koma nyanga za wolungama zidzakwezeka.

76

1 Mulungu adziwika mwa Yuda: Dzina lace limveka mwa Israyeli.

2 Msasa wace unali m'Salemu, Ndipo pokhala Iye m'Ziyoni.

3 Pomwepo anatyola mibvi ya paota; Cikopa, ndi lupanga, ndi nkhondo.

4 Inu ndinu wakuunikira, ndi womveka wakuposa mapiri muli acifwamba.

5 Olimba mtima cifunkhidwa cuma cao, agona tulo tao; Amuna onse amphamvu asowa manja ao.

6 Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo, Gareta ndi kavalo yemwe anagwa m'tulo.

7 Inu ndinu woopsa; Ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala ciriri ndani pamaso panu?

8 Mudamveketsa ciweruzo cocokera Kumwamba; Dziko lapansi linacita mantha, nilinakhala cete,

9 Pakuuka Mulungu kuti aweruze, Kuti apulumutse ofatsa onse a pa dziko lapansi.

10 Indedi, kuzaza kwace kwa munthu kudzakulemekezani; Cotsalira ca kuzazaku mudzaciletsa.

11 Windani ndipo citirani Yehova Mulungu wanu zowindazo; Onse akumzinga abwere naco copereka ca kwa Iye amene ayenera kumuopa.

12 Iye adzadula mzimu wa akulu; Akhala woopsa kwa mafumu a pa dziko lapansi.

77

1 Ndidzapfuulira kwa Mulungu ndi mau anga; Kwa Mulungu ndi mau anga, ndipo adzandicherezera khutu.

2 Tsiku la nsautso yanga ndinafuna Ambuye: Dzanja langa linatambalika usiku, losaleka; Mtima wanga unakanakutonthozedwa.

3 Ndikumbukila Mulungu ndipo ndibvutika; Ndilingalira ndipo mzimu wanga ukomoka.

4 Mundikhalitsa maso; Ndigwidwa mtima wosanena kanthu.

5 Ndinaganizira masiku akale, zaka zakalekale.

6 Ndikumbukila Nyimbo yanga, usiku; Ndilingalira mumtima mwanga; Mzimu wanga unasanthula.

7 Kodi Mulungu adzataya nthawi yonse? Osabwerezanso kukondwera nafe.

8 Cifundo cace calekeka konse konse kodi? Lonjezano lace lidatha kodi ku mibadwo yonse?

9 Kodi Mulungu waiwala kucita cifundo? Watsekereza kodi nsoni zokoma zace mumkwiyo?

10 Ndipo ndinati, Cindilaka ici; Koma ndikumbukila zaka za dzanja lamanja la Wam'mwambamwamba.

11 Ndidzakumbukila zimene adazicita Ambuye; Inde, ndidzakumbukila zodabwiza zanu zoyambira kale.

12 Ndipo ndidzalingalira nchito yanu yonse, Ndi kulingalirabe zimene munazicita Inu.

13 Mulungu, m'malo opatulika muli njira yanu; Mulungu wamkuru ndani monga Mulungu?

14 Inu ndinu Mulungu wakucita codabwiza; Munazindikiritsa mphamvu yanu mwa mitundu ya anthu.

15 Munaombola anthu anu ndi mkonowanu, Ndiwo ana a Yakobo, ndi a Yosefe.

16 Madziwo anakuonani Mulungu; Anakuonani madziwo; anacita mantha: Zozama zomwe zinanjenjemera,

17 Makongwa anatsanula madzi; Thambo lidamvetsa liu lace; Mibvi yanu yomwe inaturukira.

18 Liu la bingu lanu linatengezanatengezana; Mphezi zinaunikira ponse pali anthu; Dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.

19 Njira yanu inali m'nyanja, Koyenda Inu nku madzi akulu, Ndipo mapazi anu sanadziwika.

20 Munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa, Ndi dzanja la Mose ndi Aroni,

78

1 Tamverani, anthu anga, cilamulo canga; Cherezani khutu lanu mau a pakamwa panga.

2 Ndidzatsegula pakamwa panga mofanizira; Ndidzachula zinsinsi zoyambira kale;

3 Zimene tinazimva, ndi kuzidziwa, Ndipo makolo athu anatifotokozera.

4 Sitidzazibisira ana ao, Koma kufotokozera mbadwo ukudzawo zolemekeza za Yehova, Ndi mphamvu yace, ndi zodabwiza zace zimene anazicita.

5 Anakhazika mboni mwa Yakobo, Naika cilamulo mwa Israyeli, Ndizo analamulira atate athu, Akazidziwitse ana ao;

6 Kuti mbadwo ukudzawo udziwe, ndiwo ana amene akadzabadwa; Amene adzaimirira nadzafotokozera ana ao:

7 Ndi kuti ciyembekezo cao cikhale kwa Mulungu, Osaiwala zocita Mulungu, Koma kusunga malamulo ace ndiko.

8 Ndi kuti asange makolo ao, Ndiwo mbadwo woukirana ndi wopikisana ndi Mulungu; Mbadwo wosakonza mtima wao, Ndi mzimu wao sunakhazikika ndi Mulungu.

9 Ana a Efraimu okhala nazo zida, oponya nao mauta, Anabwerera m'mbuyo tsiku la nkhondo.

10 Sanasunga cipangano ca Mulungu, Nakana kuyenda m'cilamulo cace.

11 Ndipo anaiwala zocita Iye, Ndi zodabwiza zace zimene anawaonetsa.

12 Anacita codabwiza pamaso pa makolo ao, M'dziko la Aigupto ku cidikha ca Zoanu.

13 Anagawa nyanja nawapititsapo; Naimitsa madziwo ngati khoma.

14 Ndipo msana anawatsogolera ndi mtambo Ndi usiku wonse ndi kuunika kwa moto.

15 Anang'alula thanthwe m'cipululu, Ndipo anawamwetsa kocuruka monga m'madzi ozama.

16 Anaturukitsa mitsinje m'thanthwe, Inde anatsikitsa madzi ngati mitsinje.

17 Koma anaonjeza kuincimwira Iye, Kupikisana ndi Wam'mwambamwamba m'cipululu.

18 Ndipo anayesa Mulungu mumtimamwao Ndi kupempha cakudya monga mwa kulakalaka kwao.

19 Ndipo analankhula motsutsana ndi Mulungu; Anati, Kodi Mulungu akhoza kutikonzera podyera m'cipululu?

20 Taonani, anapanda thanthwe, ndi madzi anayendako Ndi mitsinje inasefuka; Kodi adzakhozanso kupatsa mkate? Kodi adzafunira anthu ace nyama?

21 Cifukwa cace Yehova anamva, nakwiya; Ndipo anayatsa moto pa Yakobo, Ndiponso mkwiyo unakwera pa Israyeli;

22 Popeza sanakhulupirira Mulungu, Osatama cipulumutso cace.

23 Koma analamulira mitambo iri m'mwamba, Natsegula m'makomo a kumwamba.

24 Ndipo anawabvumbitsira mana, adye, Nawapatsa tirigu wa kumwamba.

25 Yense anadya mkate wa omveka: Anawatumizira cakudya cofikira,

26 Anaombetsa m'mwamba mphepo ya kum'mawa: Natsogoza mwela ndi mphamvu yace.

27 Ndipo anawabvumbitsira nyama ngati pfumbi, Ndi mbalame zouluka ngati mcenga wa kunyanja:

28 Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao, Pozungulira pokhala iwo.

29 Potero anadya nakhuta kwambiri; Ndipo anawapatsa cokhumba iwo.

30 Asanathe naco cokhumba cao, Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,

31 Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira, Ndipo anapha mwa onenepa ao, Nagwetsa osankhika a Israyeli.

32 Cingakhale ici conse anacimwanso, Osabvomereza zodabwiza zace.

33 Potero anathera masiku ao ndi zopanda pace, Ndi zaka zao mwa mantha.

34 Pamene anawapha ndipo anamfuna Iye; Nabwerera, nafunitsitsa Mulungu,

35 Ndipo anakumbukila kuti Mulungu ndiye thanthwe lao, Ndi Mulungu Wam'mwambamwamba Mombolo wao.

36 Koma anamsyasyalika pakamwa pao, Namnamiza ndi lilime lao.

37 Popeza mtima wao sunakonzekera Iye, Ndipo sanakhazikika m'cipangano cace.

38 Koma Iye pokhala ngwa cifundo, Anakhululukira coipa, osawaononga; Nabweza mkwiyo wace kawiri kawiri, Sanautsa ukali wace wonse.

39 Ndipo anakumbukira kuti iwo ndiwo anthu; Mphepo yopita yosabweranso.

40 Kawiri kawiri nanga anapikisana ndi Iye kucigwako, Nammvetsa cisoni m'cipululu.

41 Pakuti anabwerera m'mbuyo, nayesa Mulungu, Nacepsa Woyerayo wa Israyeli.

42 Sanakumbukila dzanja lace, Tsikuli anawaombola kwa msautsi.

43 Amene anaika zizindikilo zace m'Aigupto, Ndi zodabwiza zace ku cidikha ca Zoanu;

44 Nasanduliza nyanja yao mwazi, Ndi mitsinje yao, kuti sangakhoze kumwa.

45 Anawatumizira pakati pao mitambo ya nchenche zakuwatha; Ndi acule akuwaononga.

46 Ndipo anapatsa mphuci dzinthu dzao, Ndi dzombe nchito yao.

47 Anapha mphesa zao ndi matalala, Ndi mikuyu yao ndi cisanu.

48 Naperekanso zoweta zao kwa matalala, Ndi ng'ombe zao kwa mphezi.

49 Anawatumizira mkwiyo wace wotentha, Kuzaza, ndi kupsa mtima, ndi nsautso, Ndizo gulu la amithenga ocita zoipa.

50 Analambulira mkwiyo wace njira; Sanalekerera moyo wao usafe, Koma anapereka moyo wao kumliri;

51 Ndipo anapha ana oyamba onse a mu Aigupto, Ndiwo oyamba a mphamvu yao m'mahema a Hamu:

52 Koma anaturutsa anthu ace ngati nkhosa, Nawatsogoza ngati gulu la zoweta m'cipululu.

53 Ndipo anawatsogolera mokhulupirika, Kotero kuti sanaopa; Koma nyanja inamiza adani ao.

54 Ndipo anawafikitsa ku malire a malo ace oyera, Ku phiri ili, dzanja lamanja lace lidaligula.

55 Ndipo anapitikitsa amitundu pamaso pao, Nawagawira colowa cao, ndi muyeso, Nakhalitsa mafuko a Israyeli m'mahema mwao.

56 Koma anamuyesa napikisana ndi Mulungu Wam'mwambamwamba, Osasunga mboni zace;

57 Koma anabwerera m'mbuyo, nacita zosakhulupirika monga makolo ao: Anapatuka ngati uta wolenda,

58 Ndipo anautsa mtima wace ndi malo amsanje ao, Namcititsa nsanje ndi mafano osema.

59 Pakumva ici Mulungu, anakwiya, Nanyozatu Israyeli;

60 Ndipo anacokera cokhalamo ca ku Silo, Cihemaco adacimanga mwa anthu;

61 Napereka mphamvu yace m'ukapolo, Ndi ulemerero wace m'dzanja la msautsi.

62 Naperekanso anthu ace kwa lupanga; Nakwiya naco colandira cace.

63 Moto unapsereza anyamata ao; Ndi anamwali ao sanalemekezeka.

64 Ansembe ao anagwa ndi lupanga; Ndipo amasiye ao sanacita maliro.

65 Pamenepo Ambuye anauka ngati wam'tulo; Ngati ciphona cakucita nthungululu ndi vinyo.

66 Ndipo anapanda otsutsana naye kumbuyo; Nawapereka akhale otonzeka kosatha.

67 Tero anakana hema wa Yosefe; Ndipo sanasankha pfuko la Efraimu;

68 Koma anasankha pfuko la Yuda, Phiri la Ziyoni limene analikonda.

69 Ndipo anamanga malo oyera ace ngati kaphiri, Monga dziko lapansi limene analikhazikitsa kosatha.

70 Ndipo anasankha Davide mtumiki wace, Namtenga ku makola a nkhosa:

71 Anamtenga kuja anatsata zoyamwitsa, Awete Yakobo, anthu ace, ndi Israyeli, colandira cace.

72 Potero anawaweta monga mwa mtima wace wangwiro; Nawatsogolera ndi luso la manja ace.

79

1 Mulungu, akunja alowa m'colandira canu; Anaipsa Kacisi wanu woyera; Anacititsa Yerusalemu bwinja.

2 Anapereka mitembo ya atumiki anu ikhale cakudya ca mbalame za mlengalenga, Nyama ya okondedwa anu anaipereka kwa zirombo za m'dziko.

3 Anakhetsa mwazi wao ngati madzi pozungulira Yerusalemu; Ndipo panalibe wakuwaika.

4 Takhala cotonza ca anansi athu, Ndi coseketsa ndi colalatitsa iwo akutizinga,

5 Yehova, mudzakwiya nthawi zonse kufikira liti? Nidzatentha nsanje yanu ngati moto?

6 Thirirani mkwiyo wanu pa akunja osadziwa Inu, Ndi pa maufumu osaitana pa dzina lanu.

7 Pakuti anathera Yakobo, Napasula pokhalira iye.

8 Musakumbukile moritsutsa mphulupulu za makolo athu; Nsoni zokoma zanu zitikumike msanga: Pakuti tafoka kwambiri.

9 Tithandizeni Mulungu wa cipulumutso cathu, Cifukwa ca ulemerero wa dzina lanu; Ndipo tilanditseni, ndi kutifafanizira zoipa zathu, Cifukwa ca dzina lanu.

10 Anenerenji amitundu, Ali kuti Mulungu wao? Kubwezera cilango ca mwazi wa atumiki anu umene anaukhetsa Kudziwike pakati pa amitundu pamaso pathu,

11 Kubuula kwa wandende kufike kuli Inu; Monga mwa mphamvu yanu yaikuru lolani ana a imfa atsale;

12 Ndipo anansi athu amene anatonza Inu muwabwezere cotonza cao, Kasanu ndi kawiri kumtima kwao, Ambuye.

13 Potero ife anthu anu ndi nkhosa za pabusa panu Tidzakuyamikani kosatha; Tidzafotokozera cilemekezo canu ku mibadwo mibadwo.

80

1 Mbusa wa Israyeli, cherani khutu; Inu wakutsogolera Yosefe ngati nkhosa; Inu wokhala pa akerubi, walitsani.

2 Utsani camuna canu pamaso pa Efraimu ndi Benjamini ndi Manase, Ndipo mutidzere kutipulumutsa.

3 Mutibweze, Mulungu; Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

4 Yehova, Mulungu wa makamu, Mudzakwiyira pemphero la anthu anu kufikira liti?

5 Munawadyetsa mkate wa misozi, Ndipo munawamwetsa misozi yambiri.

6 Mutiika kuti atilimbirane anzathu; Ndipo adani athu atiseka mwa iwo okha,

7 Mulungu wa makamu, mutibweze; Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

8 Mudatenga mpesa kucokera ku Aigupto: Munapitikitsa amitundu ndi kuuoka uwu.

9 Mudasoseratu pookapo, Idagwiritsa mizu yace, ndipo unadzaza dziko.

10 Mthunzi wace unaphimba mapiri, Ndi nthambi zace zikunga mikungudza ya Mulungu.

11 Unatambalitsa mphanda zace mpaka kunyanja, Ndi mitsitsi yace kufikira ku Mtsinje.

12 Munapasuliranii maphambo ace, Kotero kuti onse akupita m'njira acherako?

13 Nguruwe zocokera kuthengo ziukumba, Ndi nyama za kucidikha ziudya,

14 Bwererani, tikupemphani, Mulungu wa makamu; Suzumirani muli m'mwamba, nimupenye, ndi kuzonda mpesa uwu,

15 Ndi tsinde limene dzanja lanu lamanja linaokae Ndi mphanda munadzilimbikitsira.

16 Unapserera ndi moto, unadulidwa; Aonongeka pa kudzudzula kwa nkhope yanu.

17 Dzanja lanu likhale pa munthu wa pa dzanja lamanja lanu; Pa mwana wa munthu amene munadzilimbikitsira.

18 Potero sitidzabwerera m'mbuyo kukusiyani; Titsitsimutseni, ndipo tidzaitanira dzina lanu.

19 Mutibweze, Yehova Mulungu wa makamu; Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

81

1 Yimbitsirani Mulungu ndiye mphamvu yathu; Pfuulirani kwa Mulungu wa Yakobo.

2 Utsani Salimo, bwera nakoni kalingaka, Zeze wokondwetsa pamodzi ndi cisakasa.

3 Ombani lipenga, pokhala mwezi, Utakula mwezi, tsiku la phwando lathu.

4 Pakuti ici ndi colemba ca kwa Israyeli, Ciweruzo ca Mulungu wa Yakobo.

5 Anaciika cikhale mboni kwa Yosefe, Pakuturuka iye ku dziko la Aigupto: Komwe ndinamva cinenedwe cosadziwa ine.

6 Ndinamcotsera katundu paphewa pace: Manja ace anamasuka kucotengera.

7 Unaitana posautsika, ndipo ndinakulanditsa; Ndinakubvomereza mobisalika m'bingu; Ndinakuyesa ku madzi a Meriba.

8 Tamvani, anthu anga, ndidzakucitirani mboni; Israyeli, ukadzandimvera!

9 Kwanu kusakhale mulungu wafuma kwina; Nusagwadire mulungu wacilendo.

10 Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakukweza kukucotsa ku dziko la Aigupto; Yasamitsa pakamwa pako ndipo ndidzalidzaza.

11 Koma anthu anga sanamvera mau anga; Ndipo Israyeli sanandibvomera.

12 Potero ndinawaperekera kuuma mtima kwao, Ayende monga mwa uphungu wao wao.

13 Ha! akadandimvera anthu anga, Akadayenda m'njira zanga Israyeli!

14 Ndikadagonjetsa adani ao msanga, Ndikadabweza dzanja langa pa owasautsa.

15 Akumuda Yehova akadamgonjera mungakhale monyenga: Koma nyengo yao ikadakhala yosatha,

16 Akadawadyetsa naye tirigu wakometsetsa: Ndikadakukhutitsanso ndi uci wa m'thanthwe.

82

1 Mulungu aima mu msonkhano wa Mulungu, Aweruza pakati pa milungu.

2 Mudzaweruza mosalunjika kufikira liti, Ndi kusamalira nkhope ya oipa?

3 Weruzani osauka ndi amasiye; Weruzani molungama ozunzika ndi osowa.

4 Pulumutsani osauka ndi aumphawi: Alanditseni m'dzanja la oipa,

5 Sadziwa, ndipo sazindikira; Amayendayenda mumdima; Maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6 Ndinati Ine, Inu ndinu milungu, Ndi ana a Wam'mwambamwamba nonsenu.

7 Komatu mudzafa monga anthu, Ndipo mudzagwa monga wina wa akulu.

8 Ukani, Mulungu, weruzani dziko lapansi; Pakuti Inu mudzalandira amitundu onse.

83

1 Mulungu musakhale cete; Musakhale du, osanena kanthu, Mulungu.

2 Pakuti taonani, adani anu aphokosera: Ndipo okwiyira Inu aweramutsa mutu,

3 Apangana mocenjerera pa anthu anu, Nakhalira upo pa obisika anu.

4 Amati, Tiyeni tiwaononge asakhalenso mtundu wa anthu; Ndipo dzina la Israyeli lisakumbukikenso.

5 Pakuti anakhalira upo ndi mtima umodzi; Anacita cipangano ca pa Inu:

6 Mahema a Edomu ndi a Aismayeli; Moabu ndi Ahagara;

7 Gebala ndi Amoni ndi Amaleki; Filistiya, pamodzi ndi iwo okhala m'Turo.

8 Asuri anaphatikana nao; Anakhala dzanja la ana a Loti,

9 Muwacitire monga munacitira Midyani; Ndi Sisera, ndi Jabini ku mtsinje wa Kisoni:

10 Amene anaonongeka ku Endoro; Anakhala ngati ndowe ya kumunda.

11 Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu; Mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna:

12 Amene anati, Tilande Malo okhalamo Mulungu, akhale athu.

13 Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu; Ngati ziputu zomka ndi mphepo.

14 Monga moto upsereza nkhalango, Ndi monga lawi liyatsa mapiri;

15 Momwemo muwatsate ndi namondwe, Nimuwaopse ndi kabvumvulu wanu.

16 Acititseni manyazi pankhope pao; Kuti afune dzina lanu, Yehova.

17 Acite manyazi, naopsedwe kosatha; Ndipo asokonezeke, naonongeke:

18 Kuti adziwe kuti inu nokha, dzina lanu ndinu Yehova, Ndinu Wam'mwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

84

1 Pokhala Inu mpotikonda ndithu, Yehova wa makamu!

2 Moyo wanga ulakalaka, inde ukomokanso ndi kufuna mabwalo a Yehova; Mtima wanga ndi thupi langa zipfuulira kwa Mulungu wamoyo.

3 Mbawanso inapeza nyumba, Ndi namzeze cisa cace coikamo ana ace, Pa maguwa a nsembe anu, Yehova wa makamu, Mfumu yanga ndi Mulungu wanga,

4 Odala iwo akugonera m'nyumba mwanu; Akulemekezani cilemekezere,

5 Wodala munthu amene mphamvu yace iri mwa Inu; Mumtima mwace muli makwalala a ku Ziyoni,

6 Popyola cigwa ca kulira misozi aciyesa ca akasupe; Inde mvula: ya cizimalupsa icidzaza ndi madalitso.

7 Apita mwamphamvu naonjezapo mphamvu, Aoneka pamaso pa Mulungu m'Ziyoni.

8 Yehova Mulungu wa makamu, imvani pemphero langa: Cherani khutu, Mulungu wa Yakobo.

9 Onani, Mulungu, ndinu cikopa cathu; Ndipo penyani pa nkhope ya Wodzozedwa wanu.

10 Pakuti tsiku limodzi m'mabwalo anu likoma koposa masiku ambirimbiri akukhala pena, Kukhala inewapakhomo m'nyumba ya Mulungu wanga, Kundikonda ine koposa kugonera m'mahema a coipa,

11 Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi cikopa; Yehova adzapatsa cifundo ndi ulemerero; Sadzakaniza cokoma iwo akuyenda angwiro,

12 Yehova wa makamu, Wodala munthu wakukhulupirira Inu.

85

1 Munacita zobvomereza dziko lanu, Yehova; Munabweza ukapolo wa Yakobo.

2 Munacotsa mphulupulu ya anthu anu, Munafotsera zolakwa zao zonse.

3 Munabweza kuzaza kwanu konse; Munabwerera ku mkwiyo wanu wotentha.

4 Mutibweze, Mulungu wa cipulumutso cathu, Nimuletse udani wanu wa pa ife.

5 Kodi mudzatikwiyira nthawi zonse? Kodi mudzakhala cikwiyire mibadwo mibadwo?

6 Kodi simudzatipatsanso moyo, Kuti anthu anu akondwerere ndi Inu?

7 Tionetseni cifundo canu, Yehova, Tipatseni cipulumutso canu.

8 Ndidzamva colankhula Mulungu Yehova; Pakuti adzalankhula zamtendere ndi anthu ace, ndi okondedwa ace; Koma asabwererenso kucita zapusa.

9 Indedi cipulumutso cace ciri pafupi ndi iwo akumuopa Iye; Kuti m'dziko mwathu mukhale ulemu.

10 Cifundo ndi coonadi zakomanizana; Cilungamo ndi mtendere zapsompsonana,

11 Coonadi ciphukira m'dziko; Ndi cilungamo casuzumira ciri m'mwamba.

12 Inde Yehova adzapereka zokoma; Ndipo dziko lathu lidzapereka zipatso zace.

13 Cilungamo cidzamtsogolera; Nicidzamkonzera mapazi ace njira.

86

1 Cherani khutu lanu Yehova, mundiyankhe; Pakuti ine ndine wozunzika ndi waumphawi.

2 Sungani moyo wanga pakuti ine ndine wokondedwa wanu; Inu Mulungu wanga, pulumutsani mtumiki wanu wokhulupirira Inu.

3 Mundicitire cifundo, Ambuye; Pakuti tsiku lonse ndiitana Inu.

4 Kondwetsani moyo wa mtumiki wanu; Pakuti ndikwezera moyo wanga kwa Inu, Ambuye.

5 Pakuti fnu, Ambuye, ndinu wabwino, ndi wokhululukira, Ndi wa cifundo cocurukira onse akuitana Inu.

6 Cherani khutu pemphero langa, Yehova; Nimumvere mau a kupemba kwanga,

7 Tsiku la msauko wanga ndidzaitana Inu; Popeza mudzandibvomereza.

8 Pakati pa milungu palibe wina wonga Inu, Ambuye; Ndipo palibe nchito zonga zanu.

9 Amitundu onse mudawalenga adzadza nadzagwada pamaso panu, Ambuye; Nadzalemekeza dzina lanu.

10 Pakuti Inu ndinu wamkulu, ndi wakucita zodabwiza; Inu ndinu Mulungu, nokhanu.

11 Mundionetse njira yanu, Yehova; ndidzayenda m'coonadi canu: Muumbe mtima wanga ukhale umodzi kuti uliope dzina lanu.

12 Ndidzakuyamikani, Ambuye, Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse; Ndipo ndidzalemekeza dzina lanu nthawi zonse.

13 Pakuti cifundo canu ca pa ine ncacikuru; Ndipo munalanditsa moyo wanga kunsi kwa manda.

14 Mulungu, odzikuza andiukira, Ndi msonkhano wa anthu oopsa afuna moyo wanga, Ndipo sanaika Inu pamaso pao.

15 Koma Inu, Ambuye, ndinu Mulungu wansoni ndi wacisomo, Wosapsa mtima msanga, ndi wocurukira cifundo ndi coonadi.

16 Mundibwerere ine, ndi kundicitira cifundo; Mpatseni mtumiki wanu mphamvu yanu, Ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.

17 Mundicitire cizindikilo coti cabwino; Kuti ondida acione, nacite manyazi, Popeza Inu, Yehova, munandithandiza ndi kundisangalatsa,

87

1 Maziko ace ali m'mapiri oyera.

2 Yehova akonda zipata za Ziyoni Koposa zokhalamo zonse za Yakobo.

3 Mudzi wa Mulungu, inu, Akunenerani zakukulemekezani.

4 Ndidzachula Rahabu ndi Babulo kwa iwo ondidziwa Ine; Taonani, Filistiya ndi Turo pamodzi ndi Kusi; Uyu anabadwa komweko.

5 Ndipo adzanena za Ziyoni, Uyu ndi uyo anabadwa m'mwemo; Ndipo Wam'mwambamwamba ndiye aclzaukhazikitsa.

6 Yehova adzawerenga, polembera mitundu ya anthu. Uyu anabadwa komweko.

7 Ndipo oyimba ndi oomba omwe adzati, Akasupe ansa onse ali mwa inu.

88

1 Yehova, Mulungu wa cipulumutso canga, Ndinapfuula pamaso panu usana ndi usiku,

2 Pemphero langa lidze pamaso panu; Mundicherere khutu kukuwa kwanga:

3 Pakuti mzimu wanga wadzala nao mabvuto, Ndi moyo wanga wayandikira kumanda.

4 Anandiwerenga pamodzi nao otsikira kudzenje; Ndakhala ngati munthu wopanda mphamvu:

5 Wotayika pakati pa akufa, Ngati ophedwa akugona m'manda, Amene simuwakumbukilanso; Ndipo anawadula kusiyana ndi dzanja lanu.

6 Munandiika kunsi kwa dzenje, Kuti mdima, kozama.

7 Mkwiyo wanu utsamira pa ine, Ndipo munandizunza ine ndi mafunde anu onse.

8 Munandisiyanitsira wodziwana nane kutali; Munandiika ndiwakhalire conyansa: Ananditsekereza osakhoza kuturuka ine.

9 Diso langa lapuwala cifukwa ca kuzunzika kwanga: Ndimaitana Inu, Yehova, tsiku lonse; Nditambalitsira manja anga kwa Inu.

10 Kodi mudzacitira akufa zodabwiza? Kodi adzaukanso otisiyawo, ndi kukulemekezani?

11 Adzafotokozera cifundo canu kumanda kodi, Cikhulupiriko canu ku malo a cionongeko?

12 Zodabwiza zanu zidzadziwika mumdima kodi, Ndi cilungamo canu m'dziko la ciiwaliko?

13 Koma ndinapfuulira kwa Inu, Yehova, Ndipo pemphero langa likumika Inu mamawa.

14 Yehova mutayiranji moyo wanga? Ndi kundibisira nkhope yanu?

15 Wozunzika ine ndi wofuna kufa kuyambira ubwana wanga; Posenza zoopsa zanu, ndithedwa nzeru.

16 Kuzaza kwanu kwandimiza; Zoopsa zanu zinandiononga,

17 Zinandizungulira ngati madzi tsiku lonse; Zinandizinga pamodzi.

18 Munandicotsera kutali wondikonda ndi bwenzi langa, Odziwana nane akhala kumdima.

89

1 Ndidzayimbira zacifundo za Yehova nthawi yonse: Pakamwa panga ndidzadziwitsira cikhulupiriko canu ku mibadwo mibadwo.

2 Pakuti ndinati, Cifundo adzacimanga kosaleka; Mudzakhazika cikhulupiriko canu m'Mwamba mweni mweni.

3 Ndinacita cipangano ndi wosankhika wanga, Ndinalumbirira Davide mtumiki wanga:

4 Ndidzakhazika mbeu yako ku nthawi yonse, Ndipo ndidzamanga mpando wacifumu wako ku mibadwo mibadwo.

5 Ndipo kumwamba kudzalemekeza zodabwiza zanu, Yehova; Cikhulupiriko canunso mu msonkhano wa oyera mtima.

6 Pakuti kuli yani kuthambo timlinganize ndi Yehova? Afanana ndi Yehova ndani mwa ana a amphamvu?

7 Ndiye Mulungu, ayenera kumuopa kwambiri m'upo wa oyera mtima, Ndiye wocititsa mantha koposa onse akumzinga.

8 Yehova, Mulungu wa makamu, wamphamvu ndani wonga Inu, Yehova? Ndipo cikhulupiriko canu cikuzingani.

9 Inu ndinu wakucita ufumu pa kudzikuza kwa nyanja; Pakuuka mafunde ace muwacititsa bata.

10 Mudathyola Rahabu, monga munthu wophedwa; Munabalalitsa adani anu ndi mkono wa mphamvu yanu.

11 Kumwamba ndi kwanu, dziko lapansi lomwe ndi lanu; Munakhazika dziko lokhalamo anthu ndi kudzala kwace.

12 Munalenga kumpoto ndi kumwela; Tabora ndi Hermoni apfuula mokondwera m'dzina lanu.

13 Muli nao mkono wanu wolimba; M'dzanja mwanu muli mphamvu, dzanja lamanja lanu nlokwezeka.

14 Cilungamo ndi ciweruzo ndiwo maziko a mpando wacifumu wanu; Cifundo ndi coonadi zitsogolera pankhope panu.

15 Odala anthu odziwa liu la lipenga; Ayenda m'kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.

16 Akondwera m'dzina lanu tsiku lonse; Ndipo akwezeka m'cilungamo canu.

17 Popeza Inu ndinu ulemerero wa mphamvu yao; Ndipo potibvomereza Inu nyanga yathu idzakwezeka.

18 Pakuti cikopa cathu cifuma kwa Yehova; Ndi mfumuyathu kwa Woyera wa Israyeli.

19 Pamenepo munalankhula m'masompenya ndi okondedwa anu, Ndipo mudati, Ndasenza thandizo pa ciphona; Ndakweza wina wosankhika mwa anthu.

20 Ndapeza Davide mtumiki wanga; Ndamdzoza mafuta anga oyera.

21 Amene dzanja langa lidzakhazikika naye; Inde mkono wanga udzalimbitsa.

22 Mdani sadzamuumira mtima; Ndi mwana wa cisalungamo sadzamzunza.

23 Ndipo ndidzaphwanya omsautsa pamaso pace; Ndidzapandanso odana naye.

24 Koma cikhulupiriko canga ndi cifundo canga zidzakhala naye; Ndipo nyanga yace idzakwezeka m'dzina langa.

25 Ndipo ndidzaika dzanja lace panyanja, Ndi dzanja lamanja lace pamitsinje.

26 Iye adzandichula, ndi kuti, Inu ndinu Atate wanga, Mulungu wanga, ndi thanthwe la cipulumutso canga.

27 Inde ndidzamuyesa mwana wanga woyamba, Womveka wa mafumu a pa dziko lapansi.

28 Ndidzamsungira cifundo canga ku nthawi yonse, Ndipo cipangano canga cidzalimbika pa iye.

29 Ndidzakhalitsanso mbeu yace cikhalire, Ndi mpando wacifumu wace ngati masiku a m'mwamba.

30 Ana ace akataya cilamulo canga, Osayenda m'maweruzo anga:

31 Nakaipsa malembo anga; Osasunga malamulo anga;

32 Pamenepo ndidzazonda zolakwa zao ndi ndodo, Ndi mphulupulu zao ndi mikwingwirima.

33 Koma sindidzamcotsera cifundo canga conse, Ndi cikhulupiriko canga sicidzamsowa.

34 Sindidzaipsa cipangano canga, Kapena kusintha mau oturuka m'milomo yanga.

35 Ndinalumbira kamodzi m'ciyero canga; Sindidzanamizira Davide;

36 Mbeu yace idzakhala ku nthawi yonse, Ndi mpando wacifumu wace ngati dzuwa pamaso panga.

37 Udzakhazikika ngati mwezi ku nthawi yonse, Ndi ngati mboni yokhulupirika kuthambo.

38 Koma Inu munamtaya, nimunamkaniza, Munakwiya naye wodzozedwa wanu.

39 Munakaniza cipangano ca mtumiki wanu; Munaipsa korona wace ndi kumponya pansi,

40 Munapasula maguta ace onse; Munagumula malinga ace.

41 Onse opita panjirapa amfunkhira: Akhala cotonza ca anansi ace.

42 Munakweza dzanja lamanja la iwo omsautsa; Munakondweretsa adani ace onse.

43 Munapinditsa kukamwa kwace kwa lupanga lace, Osamuimika kunkhondo.

44 Munaleketsa kuwala kwace, Ndipo munagwetsa pansi mpando wacifumu wace.

45 Munafupikitsa masiku a mnyamata wace; Munamkuta nao manyazi.

46 Mudzabisala kosatha kufikira liti, Yehova; Ndi kuzaza kwanu kudzatentha ngati moto kufikira liti?

47 Kumbukilani kuti nthawi yanga njapafupi; Munalengeranji ana onse a anthu kwacabe?

48 Munthu ndani amene adzakhalabe ndi moyo, osaona imfa? Amene adzapulumutsa moyo wace ku mphamvu ya manda?

49 Ciri kuti cifundo canu cakale, Ambuye, Munacilumbirira Davide pa cikhulupiriko canu?

50 Kumbukilani, Ambuye, cotonzera atumiki anu; Ndicisenza m'cifuwa mwanga cacokera ku mitundu yonse yaikuru ya anthu;

51 Cimene adani anu, Yehova, atonza naco; Cimene atonzera naco mayendedwe a wodzozedwa wanu.

52 Wodalitsika Yehova ku nthawi yonse, Amen ndi Amen.

90

1 Ambuye, Inu munatikhalira mokhalamo M'mibadwo mibadwo.

2 Asanabadwe mapiri, Kapena musanalenge dziko lapansi, ndi lokhalamo anthu, Inde, kuyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha, Inu ndinu Mulungu.

3 Mubweza munthu akhale pfumbi; Nimuti, Bwererani inu, ana a anthu.

4 Pakuti pamaso panu zaka zikwi Zikhala ngati dzulo, litapita, Ndi monga ulonda wa usiku.

5 Muwatenga ngati ndi madzi akulu, akhala ngati tulo; Mamawa akhala ngati msipu waphuka.

6 Mamawa uphuka bwino; Madzulo ausenga, nuuma.

7 Pakuti tionongeka mu mkwiyo wanu; Ndipo m'kuzaza kwanu tiopsedwa.

8 Munaika mphulupulu zathu pamaso panu, Ndi zoipa zathu zobisika pounikira nkhope yanu.

9 Pakuti masiku athu onse apitirira m'ukali wanu; Titsiriza moyo wathu ngati lingaliro.

10 Masiku a zaka zathu ndiwo zaka makumi asanu ndi awiri, Kapena tikakhala nayo mphamvudi zaka makumi asanu ndi atatu; Koma teronso kukula kwao kumati cibvuto ndi copanda pace; Pakuti kumapitako msanga ndipo tithawa ife tomwe.

11 Adziwa mphamvu ya mkwiyo wanu ndani, Ndi ukali wanu monga ayenera kukuopani?

12 Mutidziwitse kuwerenga masiku athu motero, Kuti tikhale nao mtima wanzeru.

13 Bwerani, Yehova; kufikira liti? Ndipo alekeni atumiki anu.

14 Mutikhutitse naco cifundo canu m'mawa; Ndipo tidzapfuula mokondwera ndi kukondwera masiku athu onse.

15 Tikondweretseni monga mwa masiku mudatizunzawa, Ndi zaka tidaona coipa.

16 Cocita Inu cioneke kwa atumiki anu, Ndi ulemerero wanu pa ana ao.

17 Ndipo cisomo cace ca Yehova Mulungu wathu cikhale pa ife; Ndipo mutikhazikitsire ife nchito ya manja athu; Inde, nchito ya manja athu muikhazikitse.

91

1 Iye amene akhala pansi m'ngaka yace ya Wam'mwambamwamba Adzagonera mu mthunzi wa Wamphamvuyonse.

2 Ndidzati kwa Yehova, Pothawirapo panga ndi linga langa; Mulungu wanga, amene ndimkhulupirira,

3 Pakuti adzakuonjola ku msampha wa msodzi, Ku mliri wosakaza.

4 Adzakufungatira ndi nthenga zace, Ndipo udzathawira kunsi kwa mapiko ace; Coonadi cace ndico cikopa cocinjiriza.

5 Sudzaopa coopsa ca usiku, Kapena mubvi wopita usana;

6 Kapena mliri woyenda mumdima, Kapena cionongeko cakuthera usana.

7 Pambali pako padzagwa cikwi, Ndi zikwi khumi pa dzanja lamanja lako; Sicidzakuyandikiza iwe.

8 Koma udzapenya ndi maso ako, Nudzaona kubwezera cilango oipa.

9 Popeza udati, Inu Yehova, ndinu pothawirapo panga Udaika Wam'mwambamwamba cokhalamo cako;

10 Palibe coipa cidzakugwera, Ndipo colanga sicidzayandikiza hema wako.

11 Pakuti adzalamulira angelo ace za iwe, Akusunge m'njira zako zonse.

12 Adzakunyamula pa manja ao, Ungagunde phazi lako pamwala.

13 Udzaponda mkango ndi mphiri; Udzapondereza msona wa mkango ndi cinjoka:

14 Popeza andikondadi ndidzampulumutsa; Ndidzamkweza m'mwamba, papeza adziwa dzina langa.

15 Adzandipfuulira Ine ndipo ndidzamyankha; Kunsautso ndidzakhala naye pamodzi; Ndidzamlanditsa, ndi kumcitira ulemu.

16 Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri, Ndi kumuonetsera cipulumutso canga,

92

1 Nkokoma kuyamika Yehova, Ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Wam'mwambamwamba Inu:

2 Kuonetsera cifundo canu mamawa, Ndi cikhulupiriko canu usiku uli wonse.

3 Pa coyimbira ca zingwe khumi ndi pacisakasa; Pazeze ndi kulira kwace.

4 Popeza Inu, Yehova, munandikondweretsa ndi kucita kwanu, Ndidzapfuula mokondwera pa nchito ya manja anu.

5 Ha! nchito zanu nzazikuru, Yehova, Zolingalira zanu nzozama ndithu.

6 Munthu wopulukira sacidziwa; Ndi munthu wopusa sacizindikira ici;

7 Cakuti pophuka oipa ngati msipu, Ndi popindula ocita zopanda pace; Citero kuti adzaonongeke kosatha:

8 Koma Inu, Yehova, muli m'mwamba ku nthawi yonse.

9 Pakuti, taonani, adani anu, Yehova, Pakuti, taonani, adani anu adzatayika; Ocita zopanda pace onse adzamwazika.

10 Koma munakweza nyanga yanga ngati ya njati; Anandidzoza mafuta atsopano.

11 Diso langa lapenya cokhumba ine pa iwo ondilalira, M'makutu mwanga ndamva cokhumba ine pa iwo akucita zoipa akundiukira.

12 Wolungama adzaphuka ngati mgwalangwa; Adzakula ngati mkungudza wa ku Lebano.

13 Iwo ookedwa m'nyumba ya Yehova, Adzaphuka m'mabwalo a Mulungu wathu.

14 Atakalamba adzapatsanso zipatso; Adzadzazidwa ndi madzi nadzakhala abiriwiri:

15 Kulalikira kuti Yehova ngwolunjika; Iye ndiye thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe cosalungama.

93

1 Yehova acita ufumu; wadzibveka ndi ukulu; Wadzibveka Yehova, wadzimangirira mphamvu m'cuuno; Dziko lomwe lokhalamo anthu likhazikika, silidzagwedezeka.

2 Mpando wacifumu wanu ukhazikika kuyambira kale lija; Inu ndinu wosayambira ndi kale, lomwe.

3 Mitsinje ikweza, Yehova, Mitsinje ikweza mkokomo wao; Mitsinje ikweza mafunde ao.

4 Yehova Wam'mwamba ndiye wamphamvu, Wakuposa mkokomo wa madzi ambiri, Ndi mafunde olimba a nyanja.

5 Mboni zanu zibvomerezeka ndithu; Ciyero ciyenera nyumba yanu, Yehova, ku nthawi za muyaya.

94

1 Mulungu wakubwezera cilango, Yehova, Mulungu wakubwezera cilango, muoneke wowala.

2 Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi: Bwezerani odzikuza coyenera iwo.

3 Oipa adzatumpha ndi cimwemwe kufikira liti, Yehova? Oipa adzatero kufikira liti?

4 Anena mau, alankhula zawawa; Adzitamandira onse ocita zopanda pace.

5 Aphwanya anthu anu, Yehova, Nazunza colandira canu.

6 Amapha wamasiye ndi mlendo, Nawapha ana amasiye.

7 Ndipo amati, Yehova sacipenya, Ndi Mulungu wa Yakobo sacisamalira.

8 Zindikirani, opulukira inu mwa anthu; Ndipo opusa inu, mudzacita mwanzeru liti?

9 Kodi Iye wakupanga khutu ngwosamva? Kodi Iye wakuumba diso ngwosapenya?

10 Kodi Iye wakulangiza mitundu ya anthu, ndiye wosadzudzula? Si ndiye amene aphunzitsa munthu nzeru?

11 Yehova adziwa zolingalira za munthu, Kuti ziri zacabe.

12 Wodala munthu amene mumlanga, Yehova; Ndi kumphunzitsa m'cilamulo canu;

13 Kuti mumpumitse masiku oipa; Kufikira atakumbira woipa mbuna.

14 Pakuti Yehova sadzasiya anthu ace, Ndipo sadzataya colandira cace.

15 Pakuti ciweruzo cidzabwera kumka kucilungamo: Ndipo oongoka mtima onse adzacitsata.

16 Adzandiukira ndani kutsutsana nao ocita zoipa? Adzandilimbikira ndani kutsutsana nao ocita zopanda pace?

17 Akadapanda kukhala thandizo langa Yehova, Moyo wanga ukadakhala kuli cete.

18 Pamene ndinati, Litereka phazi langa, Cifundo canu, Mulungu, cinandicirikiza.

19 Pondicurukira zolingalira zanga m'kati mwanga, Zotonthoza zanu zikondweretsa moyo wanga.

20 Kodi uyenera kuyanjana ndi Inu mpando wacifumu wa kusakaza, Wakupanga cobvuta cikhale lamulo?

21 Asonkhana pamodzi pa moyo wa wolungama, Namtsutsa wa mwazi wosacimwa.

22 Koma Yehova wakhala msanje wanga; Ndi Mulungu wanga thanthwe lothawirapo ine.

23 Ndipo anawabwezera zopanda pace zao, Nadzawaononga m'coipa cao; Yehova Mulungu wathu adzawaononga.

95

1 Tiyeni tiyimbire Yehova mokondwera; Tipfuule kwa thanthwe la cipulumutso cathu.

2 Tidze naco ciyamiko pamaso pace, Timpfuulire Iye mokondwera ndi masalmo.

3 Pakuti Yehova ndiye Mulungu wamkuru; Ndi mfumu yaikuru yoposa milungu yonse.

4 Malo ozama a dziko lapansi ali m'dzanja lace; Cuma ca m'mapiri comwe ndi cace.

5 Nyanja ndi yace, anailenga; Ndipo manja ace anaumba dziko louma.

6 Tiyeni, tipembedze tiwerame; Tigwade pamaso pa Yehova, amene anatilenga:

7 Pakuti Iye ndiye Mulungu wathu, Ndipo ife ndife anthu a pabusa pace, ndi nkhosa za m'dzanja mwace. Lero, mukamva mau acel

8 Musaumitse mitima yanu, ngati ku Meriba, Ngati tsiku la ku Masa m'cipululu;

9 Pamene makolo anu anandisuntha, Anandiyesa, anapenyanso cocita Ine.

10 Zaka makumi anai mbadwo uwu unandimvetsa cisoni, Ndipo ndinati, Iwo ndiwo anthu osokerera mtima, Ndipo sadziwa njira zanga.

11 Cifukwa cace ndinalumbira mu mkwiyo wanga, Ngati adzalowa mpumulo wanga.

96

1 Myimbireni Yehova nyimbo yatsopano; Myimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

2 Myimbireni Yehova, lemekezani dzina lace; Lalikirani cipulumutso cace tsiku ndi tsiku.

3 Fotokozerani ulemerero wace mwa amitundu; Zodabwiza zace mwa mitundu yonse ya anthu.

4 Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu; Ayenera amuope koposa milungu yonse.

5 Pakuti milungu yonse ya mitundu ya anthu ndiyo mafano: Koma Yehova analenga zakumwamba.

6 Pamaso pace pali ulemu ndi ukulu: M'malo opatulika mwace muli mphamvu ndi zocititsa kaso.

7 Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu, Mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu,

8 Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lace; Bwerani naco copereka, ndipo fikani ku mabwalo ace.

9 Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa: Njenjemerani pamaso pace, inu dziko lonse lapansi.

10 Nenani mwa amitundu, Yehova acita ufumu; Dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke; Adzaweruza mitundu ya anthu molunjika.

11 Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi; Nyanja ibume mwa kudzala kwace:

12 Munda ukondwerere ndi zonse ziri m'mwemo; Pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzapfuula mokondwera;

13 Pamaso pa Yehova, pakuti akudza; Pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi: Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi cilungamo, Ndi mitundu ya anthu ndi coonadi.

97

1 Yehova acita ufumu; dziko lapansi likondwere; Zisumbu zambiri zikondwerere.

2 Pomzinga pali mitambo ndi mdima; Cilungamo ndi ciweruzo ndizo zolimbitsa mpando wacifumu wace.

3 Moto umtsogolera, Nupsereza otsutsana naye pozungulirapo,

4 Mphezi zace zinaunikira dziko lokhalamo anthu; Dziko lapansi linaona nilinagwedezeka.

5 Mapiri anasungunuka ngati sera pamaso pa Yehova, Pamaso pa Ambuye wa dziko lonse lapansi.

6 Kumwamba kulalikira cilungamo cace, Ndipo mitundu yonse ya anthu ipenya ulemerero wace.

7 Onse akutumikira fano losema, Akudzitamandira nao mafano, acite manyazi: Mgwadireni Iye, milungu yonse inu.

8 Ziyoni anamva nakondwera, Nasekerera ana akazi a Yuda; Cifukwa ca maweruzo anu, Yehova.

9 Pakuti Inu, Yehova, ndinu Wam'mwambamwamba pa dziko lonse lapansi, Ndinu wokwezeka kwakukuru pamwamba pa milungu yonse yina.

10 Inuokonda Yehova, danani naco coipa: Iye asunga moyo wa okondedwa ace; Awalanditsa m'manja mwa oipa.

11 Kuunika kufesekera wolungama, Ndi cikondwerero oongoka mtima.

12 Kondwerani mwa Yehova, olungama inu; Ndipo yamikani pokumbukila ciyero cace.

98

1 Myimbireni Yehova nyimbo yatsopano; Popeza anacita zodabwiza: Dzanja lace lamanja, mkono wace woyera, zinamcitira cipulumutso,

2 Yehova anawadziwitsira cipulumutso cace; Anaonetsera cilungamo cace pamaso pa amitundu.

3 Anakumbukila cifundo cace ndi cikhulupiriko cace ku nyumba ya Israyeli; Malekezero onse a dziko lapansi anaona cipulumutso ca Mulungu wathu.

4 Pfuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi; Kuwitsani ndi kupfuulira mokondwera; inde, yimbirani zomlemekeza.

5 Myimbireni Yehova zomlemekeza ndizeze; Ndi zeze ndi mau a salmo.

6 Pfuulani pamaso pa Mfumu Yehova, Ndi mbetete ndi liu la lipenga,

7 Nyanja Ipfuule ndi kudzala kwace; Dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhalamo;

8 Mitsinje iombe manja; Mapiri apfuule pamodzi mokondwera;

9 Pamaso pa Yehova, popeza akudza kudzaweruza dziko lapansi; Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi cilungamo, Ndi mitundu ya anthu molunjika,

99

1 Yehova ndiye mfumu; mitundu ya anthu injenjemere; Iye akhala pakati pa akerubi; dziko lapansi ligwedezeke.

2 Yehova ndiye wamkuru m'Ziyoni; Ndipo akwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.

3 Alemekeze dzina lanu lalikuru ndi loopsa; Ili ndilo loyera.

4 Ndipo mphamvu ya mfumu ikonda ciweruzo; Inu mukhazikitsa zolunjika, Mucita ciweruzo ndi cilungamo m'Yakobo.

5 Mkwezeni Yehova Mulungu wathu, Ndipo padirani poponderapo mapasa ace: Iye ndiye Woyera.

6 Mwa ansembe ace muli Mose ndi Aroni, Ndi Samueli mwa iwo akuitanira dzina lace; Anaitana kwa Yehova, ndipo Iye anawayankha.

7 Iye analankhula nao mumtambo woti njo: Iwo anasunga mboni zace ndi malembawa anawapatsa,

8 Munawayankha, Yehova Mulungu wathu: Munawakhalira Mulungu wakuwakhululukira, Mungakhale munabwezera cilango pa zocita zao.

9 Mkwezeni Yehova Mulungu wathu, Ndipo gwadirani pa phiri lace loyera; Pakuti Yehova Mulungu wathu ndiye woyera.

100

1 Pfuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

2 Tumikirani Yehova ndi cikondwerero: Idzani pamaso pace ndi kumyimbira mokondwera,

3 Dziwani kuti Yehova ndiye Mulungu; Iyeyu anatilenga, ndipo ife ndife ace; Ndife anthu ace ndi nkhosa za pabusa pace.

4 Lowani ku zipata zace ndi ciyamiko, Ndi ku mabwalo ace ndi cilemekezo: Myamikeni; lilemekezeni dzina lace.

5 Pakuti Yehova ndiye wabwino; cifundo cace cimamka muyaya; Ndi cikhulupiriko cace ku mibadwo mibadwo.

101

1 Ndidzayimba za cifundo ndi ciweruzo; Ndidzayimba zakukulemekezani Inu, Yehova.

2 Ndidzacita mwanzeru m'njira yangwiro; Mudzandidzera liti? Ndidzayenda m'nyumba mwanu ndi mtima wangwiro.

3 Sindidzaika cinthu coipa pamaso panga; Cocita iwo akupatuka padera cindiipira; Sicidzandimamatira.

4 Mtima wopulukira udzandicokera; Sindidzadziwana naye woipa.

5 Wakuneneza mnzace m'tseri ndidzamdula; Wa maso odzikuza ndi mtima wodzitama sindidzamlola.

6 Maso anga ayang'ana okhulupirika m'dziko, kuti akhale ndi Ine; Iye amene ayenda m'njira yangwiro, iyeyu adzanditumikira Ine.

7 Wakucita cinyengo sadzakhala m'kati mwa nyumba yanga; Wakunena mabodza sadzakhazikika pamaso panga.

8 Mamawa onse ndidzadula oipa onse a m'dziko; Kuduliratu onse akucita zopanda pace ku mudzi wa Yehova.

102

1 Yehova, imvani pemphero langa, Ndipo mpfuu wanga ufikire Inu.

2 Musandibisire nkhope yanu tsiku la nsautso yanga; Mundichereze khutu lanu; Tsiku limene ndiitana ine mundiyankhe msanga,

3 Popeza masiku anga akanganuka ngati utsi, Ndi mafupa anga anyeka ngati nkhuni.

4 Mtima wanga ukunga udzu wamweta, nufota; Popeza ndiiwala kudya mkate wanga.

5 Cifukwa ca liu la kubuula kwanga Mnofu wanga umamatika ku mafupa anga.

6 Ndikunga bvuwo m'cipululu; Ndikhala ngati kadzidzi wa kumabwinja.

7 Ndidikira, ndikhala ngati mbawa Iri yokha pamwamba pa tsindwi.

8 Adani anga anditonza tsiku lonse; Akundiyarukirawo alumbirira ine.

9 Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate, Ndi kusanganiza-comwera canga ndi misozi,

10 Cifukwa ca ukali wanu ndi kuzaza kwanu; Popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.

11 Masiku anga akunga mthunzi womka m'tali; Ndipo ine ndauma ngati udzu.

12 Koma Inu, Yehova, mukhalabe ku nthawi yonse; Ndi cikumbukilo canu ku mibadwo mibadwo.

13 Inu mudzauka, ndi kucitira nsoni Ziyoni; Popeza yafika nyengo yakumcitira cifundo, nyengo yoikika.

14 Pakuti atumiki anu akondwera nayo miyala yace, Nacitira cifundo pfumbi lace.

15 Pamenepo amitundu adzaopa dzina la Yehova, Ndi mafumu onse a dziko lapansi ulemerero wanu;

16 Pakuti Yehova anamanga Ziyoni, Anaoneka m'ulemerero wace;

17 Anasamalira pemphero la iwo akusowa konse, Osapepula pemphero lao.

18 Ici adzacilembera mbadwo ukudza; Ndi mtundu wa anthu umene udalengedwa udzamlemekeza Yehova.

19 Pakuti anapenya pansi ali kumwamba kuli malo ace opatulika; Yehova pokhala kumwamba anapenya dziko lapansi;

20 Kuti amve kubuula kwa wandende; Namasule ana a imfa,

21 Kuti anthu alalikire dzina la Yehova m'Ziyoni, Ndi cilemekezo cace m'Yerusalemu;

22 Posonkhana pamodzi mitundu ya anthu, Ndi maufumu kuti atumikire Yehova.

23 Iye analanda mphamvu yanga panjira; Anacepsa masiku anga.

24 Ndinati, Mulungu wanga, musandicotse pakati pa masiku anga: Zaka zanu zikhalira m'mibadwo mibadwo.

25 Munakhazika dziko lapansi kalelo; Ndipo zakumwamba ndizo nchito ya manja anu.

26 Zidzatha izi, koma Inu mukhala: Inde, zidzatha zonse ngati cabvala; Mudzazisintha ngati maraya, ndipo zidzasinthika:

27 Koma Inu ndinu yemweyo, Ndi zaka zanu sizifikira kutha.

28 Ana a atumiki anu adzakhalitsa, Ndi mbeu zao zidzakhazikika pamaso panu.

103

1 Lemekeza Yehova, moyo wanga; Ndi zonse za m'kati mwanga zilemekeze dzina lace loyera.

2 Lemekeza Yehova, moyo wanga, Ndi kusaiwala zokoma zace zonse aticitirazi:

3 Amene akhululukira mphulupulu zako zonse; Naciritsa nthenda zako zonse;

4 Amene aombola moyo wako ungaonongeke; Nakubveka korona wa cifundo ndi nsoni zokoma:

5 Amene akhutitsa m'kamwa mwako ndi zabwino; Nabweza ubwana wako unge mphungu.

6 Yehova acitira onse osautsidwa Cilungamo ndi ciweruzo.

7 Analangiza Mose njira zace, Ndi ana a Israyeli macitidwe ace.

8 Yehova ndiye wa nsoni zokoma ndi wacisomo, Wosakwiya msanga, ndi wa cifundo cocuruka.

9 Sadzatsutsana nao nthawi zanse; Ndipo sadzasunga mkwiyo wace kosatha.

10 Sanaticitira monga mwa zolakwa zathu, Kapena kutibwezera monga mwa mphulupulu zathu.

11 Pakuti monga m'mwamba mutalikira ndi dziko lapansi, Motero cifundo cace cikulira iwo akumuopa Iye.

12 Monga kum'mawa kutanimpha ndi kumadzulo, Momwemo anatisiyanitsira kutali zolakwa zathu.

13 Monga atate acitira ana ace cifundo, Yehova acitira cifundo iwo akumuopa Iye.

14 Popeza adziwa mapangidwe athu; Akumbukila kuti ife ndife pfumbi.

15 Koma munthu, masiku ace akunga udzu; Aphuka monga duwa la kuthengo.

16 Pakuti mphepo ikapitapo pakhala palibe: Ndi malo ace salidziwanso.

17 Koma cifundo ca Yehova ndico coyambira nthawi yosayamba kufikira nthawi yosatha kwa iwo akumuopa Iye, Ndi cilungamo cace kufikira kwa ana a ana;

18 Kwa iwo akusunga cipangano cace, Ndi kwa iwo akukumbukila malangizo ace kuwacita.

19 Yehova anakhazika mpando wacifumu wace Kumwamba; Ndi ufumu wace ucita mphamvu ponsepo,

20 Lemekezani Yehova, inu angelo ace; A mphamvu zolimba, akucita mau ace, Akumvera liu la mau ace.

21 Lemekezani Yehova, inu makamu ace onse; Inu atumiki ace akucita comkondweretsa Iye,

22 Lemekezani Yehova, inu, nchito zace zonse, Ponse ponse pali ufumu wace: Lemekeza Yehova, moyo wanga iwe.

104

1 Lemekeza Yehova, moyo wanga; Yehova, Mulungu wanga, Inu ndinu wamkurukuru;

2 Mubvala ulemu ndi cifumu. Amene mudzikuta nako kuunika monga ndi cobvala; Ndi kuyala thambo ngati nsaru yocinga;

3 Amene alumikiza mitanda ya zipinda zace m'madzi; Naika makongwa akhale agareta ace; Nayenda pa mapiko a mphepo;

4 Amene ayesa mphepo amithenga ace; Lawi la moto atumiki ace;

5 Anakhazika dziko lapansi pa maziko ace, Silidzagwedezeka ku nthawi yonse.

6 Mudalikuta ndi nyanja ngati ndi cobvala; Madzi anafikira pamwamba pa mapiri,

7 Pa kudzudzula kwanu anathawa; Anathawa msanga liu la bingu lanu;

8 Anakwera m'mapiri, anatsikira m'zigwa, Kufikira malo mudawakonzeratu.

9 Munaika malire kuti asapitirireko; Kuti asabwererenso kuphimba dziko lapansi.

10 Atumiza akasupe alowe m'makwawa; Ayenda pakati pa mapiri:

11 Zimamwamo nyama zonse za kuthengo; Mbidzi zipherako ludzu lao.

12 Mbalame za mlengalenga zifatsa pamenepo, Zimayimba pakati pa mitawi.

13 Iye amwetsa mapiri mocokera m'zipinda zace: Dziko lakhuta zipatso za nchito zanu.

14 Ameretsa msipu ziudye ng'ombe, Ndi zitsamba acite nazo munthu; Naturutse cakudya cocokera m'nthaka;

15 Ndi vinyo wokondweretsa mtima wa munthu, Ndi mafuta akunyezimiritsa nkhope yace, Ndi mkate wakulimbitsa mtima wa munthu.

16 Mitengo ya Mulungu yadzala ndi madzi; Mikungudza ya ku Lebano imene anaioka;

17 M'mwemo mbalame zimanga zisa zao; Pokhala cumba mpa mitengo ya mikungudza,

18 Mapiri atali ndiwo ayenera zinkhoma; Pamatanthwe mpothawirapo mbira.

19 Anaika mwezi nyengo zace; Dzuwa lidziwa polowera pace.

20 Muika mdima ndipo pali usiku; Pamenepo zituruka zirombo zonse za m'thengo.

21 Misona ya mkango ibangula potsata nyama yao, Nifuna cakudya cao kwa Mulungu.

22 Poturuka dzuwa, zithawa, Zigona pansi m'ngaka mwao.

23 Pamenepo munthu aturukira ku nchito yace, Nagwiritsa kufikira madzulo.

24 Nchito zanu zicurukadi, Yehova! Munazicita zonse mwanzeru; Dziko lapansi lidzala naco cuma canu.

25 Nyanja siyo, yaikuru ndi yacitando, M'mwemo muli zokwawa zosawerengeka; Zamoyo zazing'ono ndi zazikuru.

26 M'mwemo muyenda zombo; Ndi livyatanu amene munamlenga aseweremo.

27 Izi zonse zikulindirirani, Muzipatse cakudya cao pa nyengo yace.

28 Cimene muzipatsa zigwira; Mufumbatula dzanja lanu, zikhuta zabwino.

29 Mukabisa nkhope yanu, ziopsedwa; Mukalanda mpweya wao, zikufa, Nizibwerera kupfumbi kwao.

30 Potumizira mzimu wanu, zilengedwa; Ndipo mukonzanso nkhope ya dziko lapansi.

31 Ulemerero wa Yehova ukhale kosatha; Yehova akondwere mu nchito zace;

32 Amene apenyerera pa dziko lapansi, ndipo linjenjemera; Akhudza mapiri, ndipo afuka.

33 Ndidzayimbira Yehova m'moyo mwanga: Ndidzayimbira Mulungu wanga zomlemekeza pokhala ndiripo.

34 Pomlingirira Iye pandikonde; Ndidzakondwera mwa Yehova.

35 Ocimwa athedwe ku dziko lapansi, Ndi oipa asakhalenso. Yamika Yehova, moyo wanga. Haleluya.

105

1 Yamikani Yehova, itanirani pa dzina lace; Bukitsani mwa mitundu ya anthu zocita Iye.

2 Myimbireni, myimbireni zomlemekeza; Fotokozerani zodabwiza zace zonse.

3 Mudzitamandire ndi dzina lace loyera: Mitima yao ya iwo ofunsira Yehova ikondwere.

4 Funani Yehova, ndi mphamvu yace; Funsirani nkhope yace nthawi zonse.

5 Kumbukilani zodabwiza zace adazicita; Zizindikilo zace ndi maweruzo a pakamwa pace;

6 Inu mbeu za Abrahamu, mtumiki wace, Inu ana a Yakobo, osankhika ace.

7 Iye ndiye Yehova, Mulungu wathu; Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi.

8 Akumbukila cipangano cace kosatha, Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;

9 Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu, Ndi lumbiro lace ndi Isake;

10 Ndipo anaciimikira Yakobo, cikhale malemba, Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli.

11 Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani, Gawo la colandira cako;

12 Pokhala iwo anthu owerengeka, Inde, anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;

13 Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina, Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.

14 Sanalola munthu awasautse; Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;

15 Ndi kuti musamakhudza odzozedwa anga, Musamacitira coipa aneneri anga.

16 Ndipo anaitana njala igwere dziko; Anatyola mcirikizo wonse wa mkate.

17 Anawatsogozeratu munthu; Anamgulitsa Yosefe akhale kapolo:

18 Anapweteka miyendo yace ndi matangadza; Anamgoneka m'unyolo;

19 Kufikira nyengo yakucitika maneno ace; Mau a Yehova anamuyesa.

20 Mfumuyo anatuma munthu nammasula; Woweruza mitundu ya anthu anamtsegulira.

21 Anamuika akhale woyang'anira nyumba yace, Ndi woweruza wa pa zace zonse:

22 Amange nduna zace iye mwini, Alangize akulu ace adziwe nzeru.

23 Pamenepo Israyeli analowa m'Aigupto; Ndi Yakobo anakhala mlendo m'dziko la Hamu.

24 Ndipo anacurukitsatu mtundu wa anthu ace, Nawapatsa mphamvu yoposa owasautsa.

25 Anasanduliza mitima yao, kuti adane nao anthu ace, Kuti acite monyenga ndi atumiki ace.

26 Anatuma Mose mtumiki wace, Ndi Aroni amene adamsankha.

27 Anaika pakati pao zizindikilo zace, Ndi zodabwiza m'dziko la Hamu.

28 Anatumiza mdima ndipo kunada; Ndipo sanapikisana nao mau ace.

29 Anasanduliza madzi ao akhale mwazi, Naphanso nsomba zao.

30 Dziko lao linacuruka acule, M'zipinda zomwe za mafumu ao.

31 Ananena, ndipo inadza mitambo ya nchenche, Ndi nsabwe kufikira m'malire ao onse.

32 Anawapatsa mvula yamatalala, Lawi la moto m'dziko lao.

33 Ndipo anapanda mipesa yao, ndi mikuyu yao; Natyola mitengo kufikira m'malire ao onse.

34 Ananena, ndipo linadza dzombe Ndi mphuci, ndizo zosawerengeka,

35 Ndipo zinadya zitsamba zonse za m'dziko mwao, Zinadyanso zipatso za m'nthaka mwao.

36 Ndipo Iye anapha acisamba onse m'dziko mwao Coyambira ca mphamvu yao yonse.

37 Ndipo anawaturutsa pamodzi ndi siliva ndi golidi: Ndi mwa mafuko ao munalibe mmodzi wokhumudwa.

38 Aigupto anakondwera pakucoka iwo; Popeza kuopsa kwao kudawagwera.

39 Anayala mtambo uwaphimbe; Ndi moto uunikire usiku,

40 Anafunsa ndipo Iye anadzetsa zinziri. Nawakhuritsa mkate wakumwamba.

41 Anatsegula pathanthwe, anaturukamo madzi; Nayenda pouma ngati mtsinje.

42 Popeza anakumbukila mau ace oyera, Ndi Abrahamu mtumiki wace.

43 Potero anaturutsa anthu ace ndi kusekerera, Osankhika ace ndi kupfuula mokondwera.

44 Ndipo anawapatsa maiko a amitundu; Iwo ndipo analanda zipatso za nchito ya anthu:

45 Kuti asamalire malemba ace, Nasunge malamulo ace. Haleluya.

106

1 Haleluya. Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino: Pakuti cifundo cace ncosatha.

2 Adzafotokoza ndani nchito zamphamvu za Yehova, Adzamveketsa ndani cilemekezo cace conse?

3 Odala iwo amene asunga ciweruzo, Iye amene acita cilungamo nthawi zonse.

4 Mundikumbukile, Yehova, monga momwe mubvomerezana ndi anthu anu; Mundionetsa cipulumutso canu:

5 Kuti ndione cokomaco ca osankhika anu, Kuti ndikondwere naco cikondwerero ca anthu anu, Kuti ndidzitamandire pamodzi ndi colowa canu.

6 Talakwa pamodzi ndi makolo athu; Tacita mphulupulu, tacita coipa.

7 Makolo athu sanadziwitsa zodabwiza zanu m'Aigupto; Sanakumbukila zacifundo zanu zaunyinji; Koma anapikisana ndi Inu kunyanja, ku Nyanja Yofiira.

8 Koma anawapulumutsa cifukwa ca dzina lace, Kuti adziwitse cimphamvu cace.

9 Ndipo anadzudzula Nyanja Yofiira, niiphwa: Potero anawayendetsa mozama ngati m'cipululu.

10 Ndipo anawapulumutsa m'dzanja la iye amene anawada, Nawaombola ku dzanja la mdani.

11 Ndipo madziwo anamiza owasautsa; Sanatsala mmodzi yense.

12 Pamenepo anabvomereza mau ace; Anayimbira comlemekeza.

13 Koma anaiwala nchito zace msanga; Sanalindira uphungu wace:

14 Popeza analaka-lakatu kucidikhako, Nayesa Mulungu m'cipululu.

15 Ndipo anawapatsa copempha iwo; Koma anaondetsa mitima yao.

16 Ndipo kumisasa anacita nao nsanje Mose Ndi Aroni woyerayo wa Yehova.

17 Dziko lidayasama nilidameza Datani, Ndipo linafotsera gulu la Abiramu.

18 Ndipo m'gulu mwao mudayaka moto; Lawi lace lidapsereza oipawo.

19 Anapanga mwana wa ng'ombe ku Horebu, Nagwadira fano loyenga.

20 M'mwemo anasintha ulemerero wao Ndi fanizo la ng'ombe Yakudya msipu.

21 Anaiwala Mulungu mpulumutsi wao, Amene anacita zazikulu m'Aigupto;

22 Zodabwiza m'dziko la Hamu, Zoopsa ku Nyanja Yofiira.

23 Potero Iye adati awaononge, Pakadapanda Mose wosankhika wace, kuima pamaso pace pagamukapo, Kubweza ukali wace ungawaononge,

24 Anapeputsanso dziko lofunika, Osabvomereza mau ace;

25 Koma anadandaula m'mahema mwao, Osamvera mau a Yehova.

26 Potero anawasamulira dzanja lace, Kuti awagwetse m'cipululu:

27 Kugwetsanso mbeu zao mwa amitundu, Ndi kuwabalalitsa m'maiko maiko.

28 Ndipo anadzipatikiza ndi BaalaPeori, Nadyanso nsembe za akufa.

29 Ndipo anamkwiyitsa nazo zocita zao; Kotero kuti mliri unawagwera.

30 Pamenepo panauka Pinehasi, nacita cilango: Ndi mliriwo unaletseka.

31 Ndipo adamuyesa iye wacilungamo, Ku mibadwo mibadwo ku nthawi zonse.

32 Anautsanso mkwiyo wace ku madzi a Meriba, Ndipo kudaipira Mose cifukwa ca iwowa:

33 Pakuti anawawitsa mzimu wace, Ndipo analankhula zosayenera ndi milomo yace.

34 Sanaononga mitunduyo ya anthu, Imene Mulungu adawauza;

35 Koma anasokonekerana nao amitundu, Naphunzira nchito zao:

36 Ndipo anatumikira mafano ao, Amene anawakhalira msampha:

37 Ndipo anapereka ana ao amuna ndi akazi nsembe ya kwa ziwanda,

38 Nakhetsa mwazi wosacimwa, ndi wo mwazi wa ana ao amuna ndi akazi, Amene anawaperekera nsembe mafano a Kanani; M'mwemo analidetsa dziko ndi mwaziwo.

39 Ndipo anadziipsa nazo nchito zao, Nacita cigololo nao macitidwe ao.

40 Potero udayaka mkwiyo wa Yehova pa anthu ace, Nanyansidwa Iye ndi colowa cace.

41 Ndipo anawapereka m'manja a amitundu; Ndipo odana nao anacita ufumu pa iwo.

42 Adani ao anawasautsanso, Nawagonjetsa agwire mwendo wao.

43 Iye anawalanditsa kawiri kawiri; Koma anapikisana ndi Iye mwa uphungu wao, Ndi mphulupulu zao zinawafoketsa,

44 Koma anapenya nsautso yao, Pakumva kupfuula kwao:

45 Ndipo anawakumbukila cipangano cace, Naleza monga mwa kucuruka kwa cifundo cace.

46 Ndipo anawacitira kuti apeze nsoni Pamaso pa onse amene adawamanga ndende.

47 Tipulumutseni, Yehova, Mulungu wathu, Ndi kutisokolotsa kwa amitundu, Kuti tiyamike dzina lanu loyera, Ndi kudzitamandira naco cilemekezo canu.

48 Wodala Yehova, Mulungu wa Israyeli, Kuyambira kosayamba kufikira kosatha. Ndi anthu onse anene, Amen. Haleluya,

107

1 Yamikani Yehova pakuti Iye ndiye wabwino; Pakuti cifundo cace ncosatha.

2 Atere oomboledwa a Yehova, Amene anawaombola m'dzanja la wosautsa;

3 Nawasokolotsa kumaiko, Kucokera kum'mawa ndi kumadzulo, Kumpoto ndi kunyanja.

4 Anasokera m'cipululu, m'njira yopanda anthu; Osapeza mudzi wokhalamo.

5 Anamva njala ndi ludzu, Moyo wao unakomoka m'kati mwao.

6 Pamenepo anapfuulira kwa Yehova mumsauko mwao, Ndipo anawalanditsa m'kupsinjika kwao.

7 Ndipo anawatsogolera pa njira yolunjika, Kuti amuke ku mudzi wokhalamo.

8 Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace, Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

9 Pakuti akhutitsa mtima wolakalaka, Nadzaza mtima wanjala ndi zabwino.

10 Iwo akukhala mumdima ndi mu mthunzi wa imfa, Omangika ndi kuzunzika ndi citsulo;

11 Popeza anapikisana nao mau a Mulungu, Napeputsa uphungu wa Wam'mwambamwamba;

12 Kotero kuti anagonjetsa mtima wao ndi cobvuta; Iwowa anakhumudwa koma panalibe mthandizi.

13 Pamenepo anapfuulira kwa Yehova mumsauko mwao, Ndipo anawapulumutsa m'kupsinjika kwao.

14 Anawaturutsa mumdima ndi mu mthunzi wa imfa, Nadula zomangira zao.

15 Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace, Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

16 Popeza adaswa zitseko zamkuwa, Natyola mipiringidzo yacitsulo.

17 Anthu opusa azunzika cifukwa ca zolakwa zao, Ndi cifukwa ca mphulupulu zao.

18 Mtima wao unyansidwa naco cakudya ciri conse; Ndipo ayandikira zipata za imfa.

19 Pamenepo apfuulira kwa Yehova m'kusauka kwao, Ndipo awapulumutsa m'kupsinjika kwao.

20 Atumiza mau ace nawaciritsa, Nawapulumutsa ku cionongeko cao.

21 Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace, Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

22 Ndipo apereke nsembe zaciyamiko, Nafotokozere nchito zace ndi kupfuula mokondwera.

23 Iwo akutsikira kunyanja nalowa m'zombo, Akucita nchito zao pa madzi akuru;

24 Iwowa apenya nchito za Yehova, Ndi zodabwiza zace m'madzi ozama.

25 Popeza anena, nautsa namondwe, Amene autsa mafunde ace.

26 Akwera kuthambo, atsikira kozama; Mtima wao usungunuka naco coipaco.

27 Adzandira napambanitsa miyendo ngati munthu woledzeta, Nathedwa nzeru konse.

28 Pamenepo apfuulira kwa Yehova m'kusauka kwao, Ndipo awaturutsa m'kupsinjika kwao.

29 Asanduliza namondwe akhale bata, Kotero kuti mafunde ace atonthole.

30 Pamenepo akondwera, popeza pagwabata; Ndipo Iye awatsogolera kudooko afumko.

31 Ayamike Yehova cifukwa ca cifundo cace, Ndi zodabwiza zace za kwa ana a anthu!

32 Amkwezenso mu msonkhano wa anthu, Namlemekeze pokhala akulu.

33 Asanduliza mitsinje ikhale cipululu, Ndi akasupe a madzi akhale nthaka youma;

34 Dziko lazipatso, likhale lakhulo, Cifukwa ca coipa ca iwo okhalamo.

35 Asanduliza cipululu cikhale tha wale, Ndi dziko louma likhale akasupe a madzi.

36 Ndi apo akhalitsa anjala, Kuti amangeko mudzi wokhalamo anthu;

37 Nafese m'minda, naoke mipesa, Ndiyo vakubata zipatso zolemeza.

38 Ndipo awadalitsa, kotero kuti, acuruka kwambiri; Osacepsanso zoweta zao.

39 Koma acepanso, nawerama, Cifukwa ca cisautso, coipa ndi cisoni.

40 Atsanulira cimpepulo pa akulu, Nawasokeretsa m'cipululu mopanda njira.

41 Koma aika waumphawi pamsanje posazunzika, Nampatsa mabanja ngati gulu la nkhosa.

42 Oongoka mtima adzaciona nadzasekera; Koma cosalungama conse citseka pakamwa pace.

43 Wokhala nazo nzeru asamalire izi, Ndipo azindikire zacifundo za Yehova,

108

1 Wakhazikika mtima wanga, Mulungu; Ndidzayimba, inde ndidzayimba zolemekeza, ndiko ulemerero wanga.

2 Galamukani, cisakasa ndi zeze; Ndidzauka ndekha mamawa.

3 Ndidzakuyamikani mwa mitundu ya anthu, Yehova: Ndipo ndidzayimba zakukulemekezani mwa anthu.

4 Pakuti cifundo canu ncacikuru kupitirira kumwamba, Ndi coonadi canu kufikira mitambo.

5 Kwezekani pamwamba pa thambo, Mulungu; Ndi ulemerero wanu pamwamba pa dziko lonse lapansi.

6 Kuti okondedwa anu alanditsidwe, Pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja ndipo mutibvomereze.

7 Mulungu analankhula m'ciyero cace; ndidzakondwerera: Ndidzagawa Sekemu; ndidzayesa muyeso cigwa ca Sukoti.

8 Gileadi ndi wanga: Manase ndi wanga; Ndi Efraimu ndiye mphamvu ya mutu wanga; Yuda ndiye wolamulira wanga.

9 Moabu ndiye mkhate wanga; Pa Edomu ndidzaponya nsapato yanga; Ndidzapfuulira Filistiya,

10 Adzandifikitsa ndani m'mudzi wa m'linga? Adzanditsogolera ndani ku Edomu?

11 Si ndinu Mulungu, amene mwatitaya Osaturuka nao magulu athu?

12 Tithandizeni mumsauko; Pakuti cipulumutso ca munthu ndi cabe.

13 Mwa Mulungu tidzacita molimbika mtima: Ndipo Iye adzapondereza otisautsa.

109

1 Mulungu wa cilemekezo canga, musakhale cete;

2 Pakuti pakamwa pa woipa ndi pakamwa pa cinyengo pananditsegukira; Anandilankhulira ndi m'kamwa mwa bodza.

3 Ndipo anandizinga ndi mau a udani, Nalimbana nane kopanda cifukwa.

4 M'malo mwa cikondi canga andibwezera udani; Koma ine, kupemphera ndiko.

5 Ndipo anandisenza coipa m'malo mwa cokoma, Ndi udani m'malo mwa cikondi canga.

6 Muike munthu woipa akhale mkuru wace; Ndi mdani aime pa dzanja lamanja lace.

7 Ponenedwa mlandu wace aturuke wotsutsika; Ndi pemphero lace likhale ngati kucimwa.

8 Masiku ace akhale owerengeka; Wina alandire udindo wace.

9 Ana ace akhale amasiye, Ndi mkazi wace wamasiye.

10 Ana ace akhale amcirakuyenda ndi opemphapempha; Afunefune zosowa zao kucokera m'mabwinja mwao.

11 Wokongoletsa agwire zonse ali nazo; Ndi alendo alande za nchito yace.

12 Pasakhale munthu wakumdtira cifundo; Kapena kucitira cokoma ana ace amasiye.

13 Zidzukulu zace zidulidwe; Dzina lao lifafanizidwe mu mbadwo ukudza.

14 Mphulupulu za makolo ace zikumbukike ndi Yehova; Ndi cimo la mai wace lisafafanizidwe.

15 Zikhale pamaso pa Yehova cikhalire, Kuti adule cikumbukilo cao kucicotsera ku dziko lapansi.

16 Cifukwa kuti sanakumbukila kucita cifundo, Koma analondola wozunzika ndi waumphawi, Ndi wosweka mtima, kuti awaphe.

17 Inde, anakonda kutemberera, ndipo kudamdzera mwini; Sanakondwera nako kudalitsa, ndipo kudamkhalira kutali.

18 Anabvalanso temberero ngati maraya, Ndipo lidamlowa m'kati mwace ngati madzi, Ndi ngati mafuta m'mafupa ace.

19 Limkhalire ngati cobvala adzikuta naco, Ndi lamba limene adzimangirira nalo m'cuuno cimangirire,

20 Ici cikhale mphotho ya otsutsana nane yowapatsa Yehova, Ndi ya iwo akunenera coipa moyo wanga.

21 Koma Inu, Yehova Ambuye, mucite nane cifukwa ca dzina lanu; Ndilanditseni popeza cifundo canu ndi cabwino.

22 Pakuti ine ndine wozunzika ndi waumphawi, Ndi mtima wanga walaswa m'kati mwanga.

23 Ndamuka ngati mthunzi womka m'tali Ndiingidwa kwina ndi kwina ngati dzombe.

24 Mabondo anga agwedezeka cifukwa ca kusala; Ndi mnofu wanga waonda posowa mafuta.

25 Ndiwakhaliranso cotonza; Pakundiona apukusa mutu.

26 Ndithandizeni Yehova, Mulungu wanga: Ndipulumutseni monga mwa cifundo canu;

27 Kuti adziwe kuti ici ndi dzanja lanu; Kuti Inu Yehova munacicita.

28 Atemberere iwowa, koma mudalitse ndinu; Pakuuka iwowa adzacita manyazi, koma mtumiki wanu adzakondwera.

29 Otsutsana nane abvale manyazi, Nadzikute naco cisokonezo cao ngati ndi copfunda.

30 Ndidzayamika Yehova kwakukuru pakamwa panga; Ndi pakati pa anthu aunyinji ndidzamlemekeza.

31 Popeza adzaima pa dzanja lamanja la waumphawi Kumpulumutsa kwa iwo akuweruza koipa moyo wace.

110

1 Yehova ananena kwa Ambuye wanga, Khalani pa dzanja lamanja langa, Kufikira nditaika adani anu copondapo mapazi anu.

2 Yehova adzatumiza ndodo ya mphamvu yanu kucokera ku Ziyoni; Citani ufumu pakati pa adani anu.

3 Anthu anu adzadzipereka eni ace tsiku la camuna canu: M'moyera mokometsetsa, mobadwira tnatanda kuca, Muli nae mame a ubwana wanu.

4 Yehova walamulira, ndipo sadzasintha, Inu ndinu wansembe kosatha Monga mwa cilongosoko ca Melikizedeke.

5 Yehova pa dzanja lamanja lako Adzaphwanya mafumu tsiku la mkwiyo wace.

6 Adzaweruza mwa amitundu, Adzadzaza dziko ndi mitembo; Adzaphwanya mitu m'maiko ambiri.

7 Adzamwa ku mtsinje wa panjira; Cifukwa cace adzaweramutsa mutu wace.

111

1 Haleluya. Ndidzayamika Yehova ndi mtima wonse, Mu upo wa oongoka mtima, ndi mumsonkhano.

2 Nchito za Yehova nzazikuru, Zofunika ndi onse akukondwera nazo.

3 Cocita Iye nca ulemu, ndi ukuru: Ndi cilungamo cace cikhalitsa kosatha.

4 Anacita cokumbukitsa zodabwiza zace; Yehova ndiye wa cisomo ndi nsoni zokoma.

5 Anapatsa akumuopa Iye cakudya; Adzakumbukila cipangano cace kosatha.

6 Anaonetsera anthu ace mphamvu ya nchito zace, Pakuwapatsa colowa ca amitundu.

7 Nchito za manja ace ndizo caonadi ndi ciweruzo; Malangizo ace onse ndiwo okhulupirika.

8 Acirikizika ku nthawi za nthawi, Acitika m'coonadi ndi cilunjiko,

9 Anatumizira anthu ace cipulumutso; Analamulira cipangano cace kosatha; Dzina lace ndilo loyera ndi loopedwa.

10 Kumuopa Yehova ndiko ciyambi ca nzeru; Onse akucita cotero ali naco cidziwitso cokoma; Cilemekezo cace cikhalitsa kosatha.

112

1 Haleluya. Wodala munthu wakuopa Yehova, Wakukondwera kwambiri ndi malamulo ace,

2 Mbeu yace idzakhala yamphamvu pa dziko lapansi; Mbadwo wa oongoka mtima udzadalitsidwa.

3 M'nyumba mwace mudzakhala akatundu ndi cuma: Ndi cilungamo cace cikhala cikhalire.

4 Kuupika kuturukira oongoka mtima mumdima; Iye ndiye wacisomo; ndi wansoni ndi wolungama.

5 Wodala munthu wakudtira cifundo, nakongoletsa; Adzalimbika nao mlandu wace poweruzidwa.

6 Popeza sadzagwedezeka nthawi zonse: Wolunguna adzakumbukika ku nthawi yosatha.

7 Sadzaopa mbiri yoipa; Mtima wace ngwokhazikika, wakhulupirira Yehova.

8 Mtima wace ngwocirikizika, sadzacita mantha, Kufikira ataona cofuna iye pa iwo omsautsa.

9 Anagawagawa, anapatsa aumphawi; Cilungamo cace cikhalitsa kosatha; Nyanga yace idzakwezeka ndi ulemu.

10 Woipa adzaziona, nadzapsa mtima; Adzakukuta mano, nadzasungunuka; Cokhumba oipa cidzatayika.

113

1 Haleluya; Lemekezani, inu atumiki a Yehova; Lemekezani dzina la Yehova,

2 Lodala dzina la Yehova. Kuyambira tsopano kufikira kosatha.

3 Citurukire dzuwa kufikira kulowa kwace Lilemekezedwe dzina la Yehova.

4 Yehova akwezeka pamwamba pa amitundu onse, Ulemerero wace pamwambamwamba.

5 Akunga Yehova Mulungu wathu ndani? Amene akhala pamwamba patali,

6 Nadzicepetsa apenye Zam'mwamba ndi za pa dziko lapansi.

7 Amene autsa wosauka lrumcotsa kupfumbi, Nakweza waumphawi kumcotsa kudzala.

8 Kuti amkhalitse pamodzi ndi akulu, Pamodzi ndi akulu a anthu ace.

9 Asungitsa nyumba mkazi wosaonamwana, Akhale mai wokondwera ndi ana. Haleluya.

114

1 M'mene Israyeli anaturuka ku Aigupto, Nyumba ya Yakobo kwa anthu a cinenedwe cacilendo;

2 Yuda anakhala malo ace oyera, Israyeli ufumu wace.

3 Nyanjayo inaona, nithawa; Yordano anabwerera m'mbuyo.

4 Mapiri anatumphatumpha ngati nkhosa zamphongo, Timapiri ngati ana a nkhosa.

5 Unathawanji nawe, nyanja iwe? Unabwerereranji m'mbuyo, Yordano iwe?

6 Munatumpha-tumphiranji ngati nkhosa zamphongo, mapiri inu? Ngati ana a nkhosa, zitunda inu?

7 Unjenjemere, dziko lapansi iwe, pamaso pa Ambuye, Pamaso pa Mulungu wa Yakobo;

8 Amene anasanduliza thanthwe likhale thawale lamadzi, Nsangalabwi ikhale kasupe wamadzi.

115

1 Kwa ife ai, Yehova, kwa ife ai, Koma kwa dzina lanu patsani ulemerero, Cifukwa ca cifundo canu, ndi coonadi canu.

2 Aneneranji amitundu, Ali kuti Mulungu wao?

3 Koma Mulungu wathu ndiye ali m'mwamba; Acita ciri conse cimkonda.

4 Mafano ao ndiwo a siliva ndi golidi, Nchito za manja a anthu.

5 Pakamwa ali napo, koma osalankhula; Maso ali nao, koma osapenya;

6 Makutu ali nao, koma osamva; Mphuno ali nazo, koma osanunkhiza;

7 Manja ali nao, koma osagwira; Mapazi ali nao, koma osayenda; Kapena sanena pammero pao,

8 Adzafanana nao iwo akuwapanga; Ndi onse akuwakhulupirira,

9 Israyeli, khulupirira Yehova: Ndiye mthandizi wao ndi cikopa cao.

10 Nyumba ya Aroni, khulupirira Yehova: Ndiye mthandizi wao, ndi cikopa cao.

11 Inu akuopa Yehova, khulupirirani Yehova; Ndiye mthandizi wao ndi cikopa cao.

12 Yehova watikumbukila; adzatidalitsa: Adzadalitsa nyumba ya Israyeli; Adzadalitsa nyumba ya Aroni.

13 Adzadalitsa iwo akuopa Yehova, Ang'ono ndi akuru.

14 Yehova akuonjezereni dalitso, Inu ndi ana anu.

15 Odalitsika inu a kwa Yehova, Wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16 Kunena za kumwamba, kumwamba ndiko kwa Yehova; Koma dziko lapansi analipereka kwa ana a anthu.

17 Akufa salemekeza Yehova, Kapena ali yense wakutsikira kuli cete:

18 Koma ife tidzalemekeza Yehova Kuyambira tsopano kufikira nthawi yonse. Haleluya.

116

1 Ndimkonda, popeza Yehova amamva, Mau anga ndi kupemba kwanga.

2 Popeza amandicherera khutu lace, Cifukwa cace ndidzaitanira Iye masiku anga onse.

3 Zingwe za imfa zinandizinga, Ndi zowawa za manda zinandigwira: Ndinapeza nsautso ndi cisoni.

4 Pamenepo ndinaitana dzina la Yehova; Ndikuti, Yehova ndikupemphani landitsani moyo wanga.

5 Yehova ngwa cifundo ndi wolungama; Ndi Mulungu wathu ngwa nsoni.

6 Yehova asunga opusa; Ndidafoka ine, koma anandipulumutsa,

7 Ubwere moyo wanga ku mpumulo wako; Pakuti Yehova anakucitira cokoma.

8 Pakuti munalanditsa moyo wanga kuimfa, Maso anga kumisozi, Mapazi anga, ndingagwe.

9 Ndidzayenda pamaso pa Yehova M'dziko la amoyo.

10 Ndinakhulupirira, cifukwa cace ndinalankhula; Ndinazunzika kwambiri.

11 Pofulumizidwa mtima ndinati ine, Anthu Onse nga mabodza.

12 Ndidzabwezera Yehova ciani Cifukwa ca zokoma zace zonse anandicitira?

13 Ndidzanyamula cikho ca cipulumutso, Ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova,

14 Ndidzacitazowindazanga za kwa Yehova, Tsopano, pamaso pa anthu ace onse.

15 Imfa ya okondedwa ace Nja mtengo wace pamaso pa Yehova.

16 Ndiloleni, Yehova, indetu ndine mtumiki wanu; Ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Mwandimasulira zondimanga,

17 Ndidzapereka kwa Inu nsembe yaciyamiko, Ndipo ndidzaitanira dzina la Yehova.

18 Ndidzacita zowinda zanga za kwa Yehova, Tsopano, pamaso pa anthu ace onse;

19 M'mabwalo a nyumba ya Yehova, Pakati pa inu, Yerusalemu. Haleluya.

117

1 Lemekezani Yehova, amitundu onse; Myimbireni, anthu onse.

2 Pakuti cifundo cace ca pa ife ndi cacikuru; Ndi coonadi ca Yehova ncosatha. Haleluya.

118

1 Yamikani Yehova; pakuti Iye ndiye wabwino; Pakuti cifundo cace ncosatha.

2 Anene tsono Israyeli, Kuti cifundo cace ncosatha.

3 Anene tsono nyumba ya Aroni, Kuti cifundo cace ncosatha.

4 Anene tsono iwo akuopa Yehova, Kuti cifundo cace ncosatha.

5 M'mene ndinasautsika ndinaitanira pa Yehova; Anandiyankha Dandiika motakasuka Yehova.

6 Yehova ndi wanga; sindidzaopa; Adzandicitanji munthu?

7 Yehova ndi wanga, mwa iwo akundithandiza; M'mwemo ndidzaona cofuna ine pa iwo akundida,

8 Kuthawira kwa Yehova nkokoma Koposa kukhulupirira munthu.

9 Kuthawira kwa Yehova nkokoma Koposa kukhulupirira akulu,

10 Amitundu onse adandizinga, Zedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

11 Adandizinga, inde, adandizinga: Indedi, m'dzinala Yehova ndidzawaduladula.

12 Adandizinga ngati njuci; Anazima ngati moto waminga; Indedi, m'dzina la Yehova ndidzawaduladula.

13 Kundikankha anandikankha ndikadagwa; Koma Yehova anandithandiza.

14 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Ndipo anakhala cipulumutso canga.

15 M'mahema a olungama muli liu lakupfuula mokondwera ndi la cipulumutso:

16 Dzanja lamanja la Yehova licita mwamphamvu.

17 Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo, Ndipo ndidzafotokozera nchito za Yehova.

18 Kulanga anandilangadi Yehova: Koma sanandipereka kuimfa ai.

19 Nditsegulireni zipata za cilungamo; Ndidzalowamo, ndidzayamika Yehova.

20 Cipata ca Yehova ndi ici; Olungama adzalowamo.

21 Ndidzakuyamikani, popeza munandiyankha, Ndipo munakhala cipulumutso canga,

22 Mwala umene omangawo anaukana Wakhala mutu wa pangondya.

23 Ici cidzera kwa Yehova; Ncodabwiza ici pamaso pathu.

24 Tsiku ili ndilo adaliika Yehova; Tidzasekera ndi kukondwera m'mwemo.

25 Tikupemphani, Yehova, tipulumutseni tsopano; Tikupemphani, Yehova, tipindulitseni tsopano.

26 Wodala wakudzayo m'dzina la Yehova; Takudalitsani kocokera m'nyumba ya Yehova.

27 Yehova ndiye Mulungu, amene anatiunikira; Mangani nsembe ndi zingwe, ku nyanga za guwa la nsembe.

28 Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Ndinu Mulungu wanga, ndidzakukwezani.

29 Yamikani Yehova, pakuti Iye ndiye wabwino, Pakuti cifundo cace ncosatha.

119

1 Odala angwiro m'mayendedwe ao, Akuyenda m'cilamulo ca Yehova.

2 Odala iwo akusunga mboni zace, Akumfuna ndi mtima wonse;

3 Inde, sacita cosalungama; Ayenda m'njira zace.

4 Inu munatilamulira. Tisamalire malangizo anu ndi cangu,

5 Ha! mwenzi zitakhazikika njira zanga Kuti ndisamalire malemba anu.

6 Pamenepo sindidzacita manyazi, Pakupenyerera malamulo anu onse.

7 Ndidzakuyanrikani ndi mtima woongoka, Pakuphunzira maweruzo anu olungama.

8 Ndidzasamalira malemba anu: Musandisiye ndithu.

9 Mnyamata adzayeretsa mayendedwe ace bwanji? Akawasamalira monga mwa mau anu.

10 Ndinakufunani ndi mtima wanga wonse; Ndisasokere kusiyana nao malamulo anu.

11 Ndinawabisa mau anu mumtima mwanga, Kuti ndisalakwire Inu.

12 Inu ndinu wodala Yehova; Ndiphunzitseni malemba anu.

13 Ndinafotokozera ndi milomo yanga Maweruzo onse a pakamwa panu,

14 Ndinakondwera m'njira ya mboni zanu, Koposa ndi cuma conse,

15 Ndidzalingirira pa malangizo anu, Ndi kupenyerera mayendedwe anu.

16 Ndidzadzikondweretsa nao malemba anu; Sindidzaiwala mau anu,

17 Mucitire cokoma mtumiki wanu kuti ndikhale ndi moyo; Ndipo ndidzasamalira mau anu.

18 Munditsegulire maso, kuti ndipenye Zodabwiza za m'cilamulo canu.

19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi; Musandibisire malamulo anu.

20 Mtima wanga wasweka ndi kukhumba Maweruzo anu nyengo zonse.

21 Munadzudzula odzikuza otembereredwa, Iwo akusokera kusiyana nao malamulo anu.

22 Mundicotsere cotonza, ndi cimpepulo; Pakuti ndinasunga mboni zanu.

23 Nduna zomwe zinakhala zondineneza; Koma mtumiki wanu analingirira malemba anu.

24 Mboni zanu zomwe ndizo zondikondwetsa, Ndizo zondipangira nzeru.

25 Moyo wanga umamatika ndi pfumbi; Mundipatse moyo monga mwa mau anu.

26 Ndinafotokozera njira zanga, ndipo munandiyankha: Mundiphunzitse malemba anu.

27 Mundizindikiritse njira ya malangizo anu; Kuti ndilingalire zodabwiza zanu.

28 Moyo wanga wasungunuka ndi cisoni: Mundilimbitse monga mwa mau anu.

29 Mundicotsere njira ya cinyengo; Nimundipatse mwacifundo cilamulo canu.

30 Ndinasankha njira yokhulupirika; Ndinaika maweruzo anu pamaso, panga,

31 Ndimamatika nazo mboni zanu; Musandicititse manyazi, Yehova.

32 Ndidzathamangira njira ya malamulo anu, Mutakulitsa mtima wanga.

33 Mundiphunzitse, Yehova, njira ya malemba anu; Ndidzaisunga kufikira kutha kwace.

34 Mundizindikiritse, ndipo ndidzasunga malamulo anu; Ndidzawasamalira ndi mtima wanga wonse.

35 Mundiyendetse mopita malamulo anu; Pakuti ndikondwera m'menemo.

36 Lingitsani mtima wanga ku mboni zanu, Si ku cisiriro ai.

37 Mucititse mlubza maso anga ndisapenye zacabe, Mundipatse moyo mu njira yanu.

38 Limbitsirani mtumiki wanu mau anu, Ndiye wodzipereka kukuopani.

39 Mundipatutsire cotonza canga ndiciopaco; Popeza maweruzo anu ndi okoma.

40 Taonani, ndinalira malangizo anu; Mundipatse moyo mwa cilungamo canu.

41 Ndipo cifundo canu cindidzere, Yehova, Ndi cipulumutso canu, monga mwa mau anu.

42 Kuti ndikhale nao mau akuyankha wonditonza; Popeza ndikhulupirira mau anu.

43 Ndipo musandicotsere ndithu mau a coonadi pakamwa panga; Pakuti ndinayembekeza maweruzo anu.

44 Potero ndidzasamalira malamulo anu cisamalire Ku nthawi za nthawi.

45 Ndipo ndidzayenda mwaufulu; Popeza ndinafuna malangizo anu.

46 Ndidzalankhulanso za umboni wanu pamaso pa mafumu, Osacitapo manyazi.

47 Ndipo ndidzadzikondweretsa nao malamulo anu, Amene ndiwakonda.

48 Ndidzakwezanso manja anga ku malamulo anu, amene ndiwakonda; Ndipo ndidzalingalira pa malemba anu.

49 Kumbukilani mau a kwa mtumiki wanu, Amene munandiyembekezetsa nao.

50 Citonthozo canga m'kuzunzika kwanga ndi ici; Pakuti mau anu anandipatsa moyo.

51 Odzikuza anandinyoza kwambiri: Koma sindinapatukanso naco cilamulo canu.

52 Ndinakumbukila maweruzo anu kuyambira kale, Yehova, Ndipo ndinadzitonthoza.

53 Ndinasumwa kwakukuru, Cifukwa ca oipa akusiya cilamulo canu.

54 Malemba anu anakhala nyimbo zanga M'nyumba ya ulendo wanga,

55 Usiku ndinakumbukila dzina lanu, Yehova, Ndipo ndinasamalira cilamulo canu.

56 Ici ndinali naco, Popeza ndinasunga malangizo anu.

57 Yehova ndiye gawo langa: Ndinati ndidzasunga mau anu.

58 Ndinapemba pankhope panu ndi mtima wanga wonse: Mundicitire cifundo monga mwa mau anu.

59 Ndinaganizira njira zanga, Ndipo ndinabweza mapazi anga atsate mboni zanu.

60 Ndinafulumira, osacedwa, Kusamalira malamulo anu.

61 Anandikulunga nazo zingwe za oipa; Koma sindinaiwala cilamulo canu.

62 Pakati pa usiku ndidzauka kukuyamikani Cifukwa ca maweruzo anu olungama.

63 Ine ndine wakuyanjana nao onse akukuopani, Ndi iwo akusamalira malangizo anu.

64 Dziko lapansi lidzala naco cifundo canu, Yehova; Mundiphunzitse malemba anu.

65 Munacitira mtumiki wanu cokoma, Yehova, Monga mwa mau anu.

66 Mundiphunzitse cisiyanitso ndi nzeru; Pakuti ndinakhulupirira malamulo anu.

67 Ndisanazunzidwe ndinasokera; Koma tsopano ndisamalira mau anu.

68 Inu ndinu wabwino, ndi wakucita zabwino; Mundiphunzitse malemba anu.

69 Odzikuza anandipangira bodza: Ndidzasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.

70 Mtima wao unona ngati mafuta; Koma ine ndikondwera naco cilamulo canu.

71 Kundikomera kuti ndinazunzidwa; Kuti ndiphunzire malemba anu.

72 Cilamulo ca pakamwa panu cindikomera Koposa golidi ndi siliva zikwi zikwi.

73 Manja anu anandilenga nandiumba; Mundizindikiritse, kuti ndiphunzire malemba anu.

74 Iwo amene akuopani adzandiona ine nadzakondwera; Popeza ndayembekezera mau anu;

75 Ndidziwa kuti maweruzo anu ndiwo olungama, Yehova, Ndi kuti munandizunza ine mokhulupirika.

76 Cifundo canu cikhaletu cakunditonthoza, ndikupemphani, Monga mwa mau anu kwa mtumiki wanu.

77 Nsoni zokoma zanu zindidzere, kuti ndikhale ndi moyo; Popeza cilamulo canu cindikondweretsa.

78 Odzikuza acite manyazi, popeza anandicitira monyenga ndi bodza: Koma ine ndidzalingalira malangizo anu.

79 Iwo akuopa Inu abwere kwa ine, Ndipo adzadziwa mboni zanu.

80 Mtima wanga ukhale wangwiro m'malemba anu; Kuti ndisacite manyazi.

81 Moyo wanga unakomoka ndi kukhumba cipulumutso canu: Ndinayembekezera mau anu.

82 Maso anga anatha mphamvu ndi kukhumba mau anu, Ndikuti, Mudzanditonthoza liti?

83 Popeza ndakhala ngati thumba lofukirira; Koma sindiiwala malemba anu.

84 Masiku a mtumiki wanu ndiwo angati? Mudzaweruza liti iwo akundilondola koipa?

85 Odzikuza anandikumbira mbuna, Ndiwo osasamalira cilamulo canu.

86 Malamulo anu onse ngokhulupirika; Andilondola nalo bodza; ndithandizeni.

87 Akadandithera pa dziko lapansi; Koma ine sindinasiya malangizo anu.

88 Mundipatse moyo monga mwa cifundo canu; Ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu,

89 Mau anu aikika kumwamba, Kosatha, Yehova.

90 Cikhulupiriko canu cifikira mibadwo mibadwo; Munakhazikitsa dziko lapansi, ndipo likhalitsa.

91 Kunena za maweruzo anu alimbikira kufikira lero; Pakuti onsewa ndiwo atumiki anu.

92 Cilamulo canu cikadapanda kukhala cikondweretso canga, Ndikadatayika m'kuzunzika kwanga.

93 Sindidzaiwala malangizo anu nthawi zonse; Popeza munandipatsa nao moyo.

94 Ine ndine wanu, ndipulumutseni Pakuti ndinafuna malangizo anu.

95 Oipa anandilalira kundiononga; Koma ndizindikira mboni zanu.

96 Ndinapenya malekezero ace a ungwiro wonse; Koma lamulo lanu ndi lotakasuka ndithu.

97 Ha! Ndikondadi cilamulo canu; Ndilingiriramo ine tsiku lonse.

98 Malamulo anu andipatsa nzeru yakuposa adani anga; Pakuti akhala nane cikhalire.

99 Ndiri nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse; Pakuti ndilingalira mboni zanu.

100 Ndizindikira koposa okalamba Popeza ndinasunga malangizo anu.

101 Ndinaletsa mapazi anga njira iri yonse yoipa, Kuti ndisamalire mau anu.

102 Sindinapatukana nao maweruzo anu; Pakuti Inu munandiphunzitsa.

103 Mau anu azunadi powalawa ine! Koposa uci m'kamwa mwanga.

104 Malangizo anu andizindikiritsa; Cifukwa cace ndidana nao mayendedwe onse acinyengo,

105 Mau anu ndiwo nyali ya ku mapazi anga, Ndi kuunika kwa panjira panga,

106 Ndinalumbira, ndipo ndinatsimikiza mtima, Kuti ndidzasamalira maweruzo anu olungama.

107 Ndazunzika kwambiri: Ndipatseni moyo, Yehova, monga mwa mau anu.

108 Landirani, Yehova, zopereka zaufulu za pakamwa panga, Ndipo ndiphunzitseni maweruzo anu.

109 Moyo wanga ukhala m'dzanja langa cikhalire; Koma sindiiwala cilamulo canu.

110 Oipa anandichera msampha; Koma sindinasokera m'malangizo anu.

111 Ndinalandira mboni zanu zikhale colandira cosatha; Pakuti ndizo zokondweretsa mtima wanga.

112 Ndinalingitsa mtima wanga ucite malemba anu, Kosatha, kufikira cimatiziro.

113 Ndidana nao a mitima iwiri; Koma ndikonda cilamulo canu.

114 Inu ndinu pobisalapo panga, ndi cikopa canga; Ndiyembekezera mau anu.

115 Mundicokere ocita zoipa inu; Kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga.

116 Mundicirikize monga mwa mau anu, kuti ndikhale ndi moyo; Ndipo ndisacite manyazi pa ciyembekezo canga.

117 Mundigwirizize ndipo ndidzapulumutsidwa, Ndipo ndidzasamalira malemba anu cisamalire.

118 Mupepulaonseakusokeram'malemba anu; Popeza cinyengo cao ndi bodza.

119 Mucotsa oipa onse a pa dziko lapansi ngati mphala: Cifukwa cace ndikonda mboni zanu.

120 Thupi langa linjenjemera ndi kuopa Inu; Ndipo ndicita mantha nao maweruzo anu.

121 Ndinacita ciweruzo ndi cilungamo; Musandisiyira akundisautsa.

122 Mumkhalire cikole mtumiki wanucimkomere; Odzikuza asandisautse.

123 Maso anga anatha mphamvu pafuna cipulumutso canu, Ndi mau a cilungamo canu.

124 Mucitire mtumiki wanu monga mwa cifundo canu, Ndipo ndiphunzitseni malemba anu,

125 Ine ndine mtumiki wanu, ndizindikiritseni; Kuti ndidziwe mboni zanu.

126 Yafika nyengo yakuti Yehova acite kanthu; Pakuti anaswa cilamulo canu.

127 Cifukwa cace ndikonda malamulo anu Koposa golidi, Inde golidi woyengeka,

128 Cifukwa cace ndiyesa ngolunjika malangizo anu onse akunena zonse; Koma ndidana nazo njira zonse zonyenga.

129 Mboni zanu nzodabwiza; Cifukwa cace moyo wanga uzisunga,

130 Potsegulira mau anu paunikira; Kuzindikiritsa opusa.

131 Ndinatsegula pakamwa panga, ndi kupuma wefu wefu; Popeza ndinakhumba malamulo anu.

132 Munditembenukire, ndi kundicitira cifundo, Monga mumatero nao akukonda dzina lanu.

133 Kfiazikitsanimapaziangam'mau anu; Ndipo zisandigonjetse zopanda pace ziri zonse.

134 Mundiombole ku nsautso ya munthu: Ndipo ndidzasamalira malangizo anu.

135 Muwalitse nkhope yanu pa mtumiki wanu; Ndipo mundiphunzitse malemba anu.

136 Maso anga atsitsa mitsinje ya madzi, Popeza sasamalira cilamulo canu.

137 Inu ndinu wolungama, Yehova, Ndipo maweruzo anu ndiwo olunjika.

138 Mboni zanuzo mudazilamulira Ziri zolungama ndi zokhulupirika ndithu.

139 Cangu canga cinandithera, Popeza akundisautsa anaiwala mau anu.

140 Mau anu ngoyera ndithu; Ndi mtumiki wanu awakonda.

141 Wamng'ono ine, ndi wopepulidwa; Koma sindiiwala malemba anu.

142 Cilungamo canu ndico cilungamo cosatha; Ndi cilamulo canu ndico coonadi.

143 Kusautsika ndi kupsinjika kwandigwera; Koma malamulo anu ndiwo ondikondweretsa ine.

144 Mboni zanu ndizo zolungama kosatha; Mundizindikiritse izi, ndipo ndidzakhala ndi moyo.

145 Ndinaitana ndi mtima wanga wonse; mundiyankhe, Yehova; Ndidzasunga malemba anu.

146 Ndinaitanira Inu; ndipulumutseni, Ndipo ndidzasamalira mboni zanu.

147 Ndinapfuula kusanace: Ndinayembekezera mau anu.

148 Maso anga anakumika malonda a usiku, Kuti ndilingirire mau anu.

149 Imvani liu langa monga mwa cifundo canu; Mundipatse moyo monga mwa kuweruza kwanu, Yehova.

150 Otsata zaciwembu andiyandikira; Akhala kutali ndi cilamulo canu.

151 Inu muli pafupi, Yehova; Ndipo malamulo anu onse ndiwo coonadi,

152 Kuyambira kale ndinadziwa mu mboni zanu, Kuti munazikhazika kosatha,

153 Penyani kuzunzika kwanga, nimundilanditse; Pakuti sindiiwala cilamulo canu.

154 Mundinenere mlandu wanga, nimundiombole; Mundipatse moyo monga mwa mau anu.

155 Cipulumutso citalikira oipa; Popeza safuna malemba anu.

156 Zacifundo zanu ndi zazikuru, Yehova; Mundipatse moyo monga mwa maweruzo anu.

157 Ondilondola ndi ondisautsa ndiwoambiri; Koma sindinapatukana nazo mboni zanu.

158 Ndinapenya ocita monyenga, ndipo ndinanyansidwa nao; Popeza sasamalira mau anu.

159 Penyani kuti ndikonda malangizo anu; Mundipatse moyo, Yehova, monga mwa cifundo canu.

160 Ciwerengero ca mau anu ndico coonadi; Ndi maweruzo anu olungama onse akhala kosatha.

161 Nduna zinandilondola kopanda cifukwa; Koma mtima wanga ucita mantha nao mau anu.

162 Ndikondwera nao mau anu, Ngati munthu wakupeza zofunkha zambiri.

163 Ndidana nalo bodza ndi kunyansidwa nalo; Koma ndikonda cilamulo canu.

164 Ndikulemekezani kasanu ndi kawiri, tsiku limodzi, Cifukwa ca maweruzo anu alungama.

165 Akukonda cilamulo canu ali nao mtendere wambiri; Ndipo alibe cokhumudwitsa.

166 Ndinayembekeza cipulumutso canu, Yehova, Ndipo ndinacita malamulo anu.

167 Moyo wanga unasamalira mboni zanu; Ndipo ndizikonda kwambiri.

168 Ndinasamalira malangizo anu ndi mboni zanu; Popeza njira zanga zonse ziri pamaso panu,

169 Kupfuula kwanga kuyandikire pamaso pano, Yehova; Mundizindikiritse monga mwa mau anu.

170 Kupemba kwanga kudze pamaso panu; Mundilanditse monga mwa mau anu.

171 Milomo yanga iturutse cilemekezo; Popeza mundiphunzitsa malemba anu.

172 Lilime langa liyimbire mau anu; Pakuti malamulo anu onse ndiwo olungama.

173 Dzanja lanu likhale lakundithandiza Popezandinasankha malangizo anu.

174 Ndinakhumba cipulumutso canu, Yehova; Ndipo cilamulo canu ndico condikondweretsa.

175 Mzimu wanga ukhale ndi moyo, ndipo udzakulemekezani; Ndipo maweruzo anu andithandize.

176 Ndinasocera ngati nkhosa yotayika; funani mtumiki wanu; Pakuti sindiiwala malamulo anu.

120

1 Ndinapfuulira kwa Yehova mu msauko wanga, Ndipo anandibvomereza,

2 Yehova, landitsani moyo wanga ku milomo ya mabodza, Ndi ku lilime lonyenga.

3 Adzakuninkhanji, adzakuonjezeranji, Lilime lonyenga iwe?

4 Mibvi yakuthwa ya ciphona. Ndi makara tsanya.

5 Tsoka ine, kuti ndiri mlendo m'Meseke, Kuti ndigonera m'mahema a Kedara!

6 Moyo wanga unakhalitsa nthawi Pamodzi ndi iye wakudana nao mtendere.

7 Ine ndikuti, Mtendere; Koma polankhula ine, iwowa akuti, Nkhondo.

121

1 Ndikweza maso anga kumapiri: Thandizo langa lidzera kuti?

2 Thandizo langa lidzera kwa Yehova, Wakulenga zakumwamba ndi dziko lapansi.

3 Sadzalola phazi lako literereke: Iye amene akusunga sadzaodzera.

4 Taonani, wakusunga Israyea Sadzaodzera kapena kugona.

5 Yehova ndiye wakukusunga; Yehova ndiye mthunzi wako wa ku dzanja lako lamanja.

6 Dzuwa silidzawamba usana, Mwezi sudzakupanda usiku.

7 Yehova adzakusunga kukucotsera zoipa ziri zonse; Adzasunga moyo wako.

8 Yehova adzasungira kuturuka kwako ndi kulowa kwako, Kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

122

1 Ndinakondwera m'mene ananena nane, Tiyeni ku nyumba ya Yehova.

2 Mapazi athu alinkuima M'zipata zanu, Yerusalemu.

3 Yerusalemu anamangidwa Ngati mudzi woundana bwino:

4 Kumene akwerako mafuko, ndiwo mafuko a Yehova; Akhale mboni ya kwa Israyeli, Ayamike dzina la Yehova.

5 Pakuti pamenepo anaika mipando ya ciweruzo, Mipando ya nyumba ya Davide.

6 Mupempherere mtendere wa Yerusalemu; Akukonda inu adzaona phindu.

7 M'linga mwako mukhale mtendere, M'nyumba za mafumu mukhale phindu.

8 Cifukwa ca abale anga ndi mabwenzi anga, Ndidzanena tsopano, Mukhale mtendere mwa inu.

9 Cifukwa ca nyumba ya Yehova Mulungu wathu Ndidzakufunira zokoma,

123

1 Ndikweza maso anga kwa Inu, Kwa Inu wakukhala kumwamba.

2 Taonani, monga maso a anyamata ayang'anira dzanja la ambuye ao, Monga maso a adzakazi ayang'anira dzanja la mbuye wao wamkazi: Momwemo maso athu ayang'anira Yehova Mulungu wathu, Kufikira aticitira cifundo.

3 Muticitire cifundo, Yehova, muticitire cifundo; Pakuti takhuta kwambiri ndi mnyozo.

4 Moyo wathu wakhuta ndithu Ndi kuseka kwa iwo osasowa kanthu, Ndi mnyozo wa odzikuza.

124

1 Akadapanda kukhala nafe Yehova, Anene tsono Israyeli;

2 Akadapanda kukhala nafe Yehova, Pakutiukira anthu:

3 Akadatimeza amoyo, Potipsera mtima wao.

4 Akadatimiza madziwo, Mtsinje ukadapita pa moyo wathu;

5 Madzi odzikuza akadapita pa moyo wathu.

6 Alemekezedwe Yehova, Amene sanatipereka kumano kwao tikhale cakudya cao.

7 Moyo wathu unaonjoka ngati mbalame mu msampha wa msodzi; Msampha unatyoka ndi ife tinaonioka.

8 Thandizo lathu liri m'dzina la Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

125

1 Iwo akukhulupirira Yehova Akunga phiri la Ziyoni, losasunthika, likhazikika kosatha,

2 Monga mapiri azinga Yerusalemu, Momwemo Yehova azinga anthu ace, Kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

3 Pakuti ndodo yacifumu ya coipa siidzapumula pa gawo la olungama; Kuti olungama asaturutse dzanja lao kucita cosalungama,

4 Citirani cokoma, Yehova, iwo okhala okoma; Iwo okhala oongoka mumtima mwao.

5 Koma iwo akupatuka kutsata njira zao zokhotakhota, Yehova adzawacotsa pamodzi ndi ocita zopanda pace. Mtendere ukhale pa Israyeli.

126

1 Pobweza Yehova ukapolo wa Ziyoni, Tinakhala ngati anthu akulota.

2 Pamenepo pakamwa pathu panadzala ndi kuseka, Ndi lilime lathu linapfuula mokondwera; Pamenepo anati mwa amitundu, Yehova anawacitira iwo zazikuru,

3 Yehova anaticitira ife zazikuru; Potero tikhala okondwera.

4 Bwezani ukapolo wathu, Yehova, Ngati mitsinje ya ku Mwera.

5 Akubzala ndi misozi adzatuta ndi kupfuula mokondwera.

6 Iye amene ayendayenda nalira, ponyamula mbeu yakufesa; Adzabweranso ndithu ndi kupfuula mokondwera, alikunyamula mitolo yace.

127

1 Akapanda kumanga nyumba Yehova, Akuimanga agwiritsa nchito cabe; Akapanda kusunga mudzi Yehoya, Mlonda adikira cabe.

2 Kuli cabe kwa inu Rulawirira mamawa ndi kusagonerapo madzulo, Kudya mkate wosautsa kuupeza; Kuli tero kuti izi apatsa okondedwa ace ngati m'tulo.

3 Taonani ana ndiwo colandira ca kwa Yehova; Cipatso ca m'mimba ndico mphotho yace.

4 Ana a ubwana wace wa munthu Akunga mibvi m'dzanja lace la ciphona.

5 Wodala munthu amene anadzaza nayo phodo lace: Sadzacita manyazi iwo, Pakulankhula nao adani kucipata.

128

1 Wodala yense wakuopa Yehova, Wakuyenda m'njira zace.

2 Pakuti udzadya za nchito ya manja ako; Wodala iwe, ndipo kudzakukomera.

3 Mkazi wako adzanga mpesa wopatsa m'mbali za nyumba yako; Ana ako adzanga timitengo ta azitona pozinga podyera pako.

4 Taonani, m'mwemo adzadalitsika Munthu wakuopa Yehova.

5 Yehova adzakudalitsa ali m'Ziyoni Ndipo udzaona zokoma za Yerusalemu masiku onse a moyo wako.

6 Inde, udzaona zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israyeli.

129

1 Anandisautsa kawiri kawiri kuyambira ubwana wanga, Anene tsono Israyeli;

2 Anandisautsa kawiri kawiri kuyambira ubwana wanga; Koma sanandilaka.

3 Olima analima pamsana panga; Anatalikitsa mipere yao.

4 Yehova ndiye wolungama; Anadulatu zingwe za oipa.

5 Acite manyazi nabwerere m'mbuyo. Onse akudana naye Ziyoni.

6 Akhale ngati udzu womera patsindwi, Wakufota asanauzule;

7 Umene womweta sadzaza nao dzanja lace, Kapena womanga mitolo sakupatira manja.

8 Angakhale opitirirapo sanena, Dalitso la Mulungu likhale pa inu; Tikudalitsani m'dzina la Yehova.

130

1 M'mozamamo ndinakupfuulirani, Yehova.

2 Ambuye, imvani liu langa; Makutu anu akhale cimverere Mau a kupemba kwanga.

3 Mukasunga mphulupulu, Yehova, Adzakhala ciriri ndani, Ambuye?

4 Koma kwa Inu kuli cikhululukiro, Kuti akuopeni.

5 Ndilindira Yehova, moyo wanga ulindira, Ndiyembekeza mau ace.

6 Moyo wanga uyang'anira Ambuye, Koposa alonda matanda kuca; Inde koposa alonda matanda kuca.

7 Israyeli, uyembekezere Yehova; Cifukwa kwa Yehova kuli cifundo, Kwaonso kucurukira ciombolo.

8 Ndipo adzaombola Israyeli Ku mphulupulu zace zonse.

131

1 Yehova, mtima wanga sunadzikuza Ndi maso anga sanakwezeka; Ndipo sindinatsata zazikuru, Kapena zodabwiza zondiposa.

2 Indedi, ndinalinganiza ndi kutontholetsa moyo wanga; Ngati mwana womletsa kuyamwa amace, Moyo wanga ndiri nao ngati mwana womletsa kuyamwa.

3 Israyeli, uyembekezere Yehova, Kuyambira tsopano kufikira kosatha.

132

1 Yehova, kumbukilani Davide Kuzunzika kwace konse;

2 Kuti analumbira Yehova, Nawindira Wamphamvuyo wa Yakobo, ndi kuti,

3 Ngati ndidzalowa pakhomo pa nyumba yanga, Ngati ndidzakwera pa kama logonapo;

4 Ngati ndidzalola maso anga agone, Kapena zikope zanga ziodzere;

5 Kufikira nditapezera Yehova malo, Cokhalamo Wamphamvuyo wa Yakobo?

6 Taonani, tinacimva m'Efrata; Tinacipeza ku cidikha ca kunkhalango.

7 Tidzalowa mokhalamo Iye; Tidzagwadira ku mpando wa mapazi ace.

8 Ukani, Yehova, lowani ku mpumulo wanu; Inu ndi hema wa mphamvu yanu,

9 Ansembe anu abvale cilungamo; Ndi okondedwa anu apfuule mokondwera.

10 Cifukwa ca Davide mtumiki wanu Musabweze nkhope ya wodzozedwa wanu.

11 Yehova analumbira Davide zoona; Sadzalibweza; ndi kuti, Wa iwo okhala zipatso za thupi lako ndidzaika pa mpando wacifumu wako.

12 Ana ako akasunga cipangano canga Ndi mboni yanga imene ndidzawaphunzitsa, Ana aonso adzakhala pa mpando wanu ku nthawi zonse,

13 Pakuti Yehova anasankha Ziyoni; Analikhumba likhale pokhala pace; ndi kuti,

14 Pampumulo panga mpano posatha: Pano ndidzakhala; pakuti ndakhumbapo.

15 Ndidzadalitsatu cakudya cace; Aumphawi ace ndidzawakhutitsa ndi mkate.

16 Ndipo ansembe ace ndidzawabveka ndi cipulumutso: Ndi okondedwa ace adzapfuulitsa mokondwera.

17 Apo ndidzaphukitsira Davide nyanga; Ndak onzeraru wodzozedwa wanga nyali.

18 Ndidzawabvekaadani ace ndi manyazi Koma pa iyeyu korona wace adzambveka.

133

1 Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu Kuti abale akhale pamodzi!

2 Ndiko ngati mafuta a mtengo wace pamutu, Akutsikira ku ndebvu, Inde ku ndebvu za Aroni; Akutsikira ku mkawo wa zobvala zace

3 Ngati mame a ku Hermoni, Akutsikira pa mapiri a Ziyoni: Pakuti pamenepo Yehova analamulira dalitsolo, Ndilo moyo womka muyaya,

134

1 Taonani, lemekezani Yehova, atumiki a Yehova inu nonse, Akuimirira m'nyumba ya Yehova usiku,

2 Kwezani manja anu ku malo oyera, Nimulemekeze Yehova.

3 Yehova, ali m'Ziyoni, akudalitseni; Ndiye amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi.

135

1 Haleluya; Lemekezani dzina la Yehova; Lemekezani inu atumiki a Yehova:

2 Inu akuimirira m'nyumba ya Yehova, M'mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

3 Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino; Muyimbire zolemekeza dzina lace; pakuti nkokondweretsa kutero.

4 Pakuti Yehova anadzisankhira Yakobo, Israyeli, akhale cuma cace ceni ceni.

5 Pakuti ndidziwa kuti Yehova ndi wamkuru, Ndi Ambuye wathu aposa milungu yonse.

6 Ciri conse cimkonda Yehova acicita, Kumwamba ndi pa dziko lapansi, m'nyanja ndi mozama monse.

7 Akweza mitambo icokere ku malekezero a dziko lapansi; Ang'animitsa mphezi zidzetse mvula; Aturutsa mphepo mosungira mwace.

8 Anapanda oyamba a Aigupto, Kuyambira munthu kufikira zoweta.

9 Anatumiza zizindikilo ndi zodabwiza pakati pako, Aigupto iwe, Pa Farao ndi pa omtumikira onse.

10 Ndiye amene anapanda amitundu ambiri. Napha mafumu amphamvu;

11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ndi Ogi mfumu ya Basana, Ndi maufumu onse a Kanani:

12 Ndipo anapereka dziko lao likhale cosiyira, Cosiyira ca kwa Israyeli anthu ace.

13 Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha; Cikumbukilo canu, Yehova, kufikira mibadwo mibadwo.

14 Pakuti Yehova adzaweruza anthu ace, Koma adzaleka atumiki ace.

15 Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golidi, Nchito ya manja a anthu.

16 Pakamwa ali napo koma osalankhula; Maso ali nao, koma osapenya;

17 Makutu ali nao, koma osamva; Inde, pakamwa pao palibe mpweya.

18 Akuwapanga adzafanana nao; Inde, onse akuwakhulupirira.

19 A nyumba ya Israyeli inu, lemekezani Yehova: A nyumba ya Aroni inu, lemekezani Yehova:

20 A nyumba ya Levi inu, lemekezani Yehova: Inu akuopa Yehova, lemekezani Yehova.

21 Alemekezedwe Yehova kucokera m'Ziyoni, Amene akhala m'Yerusalemu. Haleluya,

136

1 Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino: Pakuti cifundo cace ncosatha.

2 Yamikani Mulungu wa milungu: Pakuti cifundo cace ncosatha.

3 Yamikani Mbuye wa ambuye: Pakuti cifundo cace ncosatha.

4 Amene yekha acita zodabwiza zazikuru: Pakuti cifundo cace ncosatha.

5 Amene analenga zakumwamba mwanzeru: Pakuti cifundo cace ncosatha.

6 Amene anayala dziko lapansi pamwamba pa madzi: Pakuti cifundo cace ncosatha.

7 Amene analenga miuni yaikuru: Pakuti cifundo cace ncosatha.

8 Dzuwa liweruze usana: Pakuti cifundo cace ncosatha.

9 Mwezi ndi nyenyezi ziweruze usiku; Pakuti cifundo cace ncosatha.

10 Iye amene anapandira Aaigupto ana ao oyamba: Pakuti cifundo cace ncosatha.

11 Naturutsa Israyeli pakati pao; Pakuti cifundo cace ncosatha.

12 Ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka: Pakuti cifundo cace ncosatha.

13 Amene anagawa magawo Nyanja Yofiira: Pakuti cifundo cace ncosatha.

14 Napititsa Israyeli pakati pace; Pakuti cifundo cace ncosatha.

15 Nakhutula Farao ndi khamu lace m'Nyanja Yofiira: Pakuti cifundo cace ncosatha.

16 Amene anatsogolera anthu ace m'cipululu: Pakuti cifundo cace ncosatha.

17 Amene anapanda mafumu akulu: Pakuti cifundo cace ncosatha,

18 Ndipo anawapha mafumu omveka: Pakuti cifundo cace ncosatha.

19 Sihoni mfumu ya Aamori; Pakuti cifundo cace ncosatha.

20 Ndi ogi mfumu ya Basana: Pakuti cifundo cace ncosatha.

21 Ndipo anaperekadzikolaolikhale cosiyira; Pakuti cifundo cace ncosatha.

22 Cosiyira ca kwa Israyeli mtumiki wace; Pakuti cifundo cace ncosatha.

23 Amene anatikumbukila popepuka ife; Pakuti cifundo cace ncosatha.

24 Natikwatula kwa otisautsa; Pakuti cifundo cace ncosatha.

25 Ndiye wakupatsa nyama zonse cakudya; Pakuti cifundo cace ncosatha.

26 Yamikani Mulungu wa kumwamba, Pakuti cifundo cace ncosatha.

137

1 Ku mitsinje ya ku Babulo, Kumeneko tinakhala pansi, inde tinalira, Pokumbukila Ziyoni.

2 Pa msondodzi uli m'mwemo Tinapacika mazeze athu.

3 Popeza pamenepo akutigwirawo anatifunsa nyimbo, Ndipo akutizunza anafuna tisekere, Ndi kuti, Mutiyimbire nyimbo imodzi ya ku Ziyoni.

4 Tidati, Tidzayimba bwanji nyimbo ya Yehova M'dziko lacilendo?

5 Ndikakuiwalani, Yerusalemu, Dzanja lamanja langa liiwale luso lace.

6 Lilime langa limamatike ku nsaya zanga, Ndikapanda kukumbukila inu; Ndikapanda kusankha Yerusalemu Koposa cimwemwe canga copambana.

7 Yehova, kumbukilani ana a Edomu Tsiku la Yerusalemu; Amene adati, Gamulani, gamulani, Kufikira maziko ace.

8 Mwana wamkazi wa ku Babulo, iwe amene udzapasulidwa; Wodala iye amene adzakubwezera cilango Monga umo unaticitira ife.

9 Wodala iye amene adzagwira makanda ako, Ndi kuwaphwanya pathanthwe.

138

1 Ndidzakuyamikani ndi mtima wangawonse; Ndidzayimba zakukulemekezani patsogolo pa milungu,

2 Ndidzagwadira kuloza ku Kacisi wanu woyera, Ndi kuyamika dzina lanu, Cifukwa ca cifundo canu ndi coonadi canu; Popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.

3 Tsiku loitana ine, munandiyankha, Munandilimbitsa ndi mphamvu m'moyo mwanga.

4 Mafumu onse a pa dziko lapansi adzakuyamikani, Yehova, popeza adamva mau a pakamwa panu.

5 Ndipo adzayimbira njira za Yehova; Pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukuru.

6 Angakhale Yehova ngwokwezeka, apenyanso wopepukayo; Koma wodzikuza amdziwira kutali.

7 Ndingakhale ndiyenda pakati pa nsautso, mudzandipatsa moyo; Mudzatambasula dzanja lanu pa mkwiyo wa adani anu, Ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.

8 Yehova adzanditsirizira za kwa ine: Cifundo canu, Yehova, cifikira ku nthawi zonse: Musasiye nchito za manja anu.

139

1 Munandisanthula, Yehova, nimundidziwa.

2 Inumudziwakukhalakwangandi kuuka kwanga, Muzindikira lingaliro langa muli kutali.

3 Muyesa popita ine ndi pogona ine, Ndi njira zanga zonse muzolowerana nazo.

4 Pakuti asanafike mau pa lilime langa, Taonani, Yehova, muwadziwa onse.

5 Munandizinga kumbuyo ndi kumaso, Nimunaika dzanja lanu pa ine.

6 Kudziwa ici kundilaka ndi kundidabwiza: Kundikhalira patali, sindifikirako.

7 Ndidzapita kuti kuzembera mzimu wanu? Kapena ndidzathawira kuti kuzembera nkhope yanu?

8 Ndikakwera kumka kumwamba, muli komweko; Kapena ndikadziyalira ku Gehena, taonani, muli komweko.

9 Ndikadzitengera mapiko a mbanda kuca, Ndi kukhala ku malekezero a nyanja;

10 Kungakhale komweko dzanja lanu lidzanditsogolera, Nilidzandigwira dzanja lanu lamanja.

11 Ndipo ndikati, Koma mdima undiphimbe, Ndi kuunika kondizinga kukhale usiku:

12 Ungakhale mdima sudetsa pamaso panu, Koma usiku uwala ngati usana: Mdima ukunga kuunika.

13 Pakuti Inu munalenga imso zanga; Munandiumba ndisanabadwe ine.

14 Ndikuyamikani cifukwa kuti cipangidwe canga ncoopsa ndi codabwiza; Nchito zanu nzodabwiza; Moyo wanga ucidziwa ici bwino ndithu.

15 Thupi langa silinabisikira Inu popangidwa ine mobisika, Poombedwa ine monga m'munsi mwace mwa dziko lapansi.

16 Ndisanaumbidwe ine maso anu anandipenya, Ziwalo zanga zonse zinalembedwa m'buku mwanu, Masiku akuti ziumbidwe, Pakalibe cimodzi ca izo.

17 Potero, Mulungu, ndiziyesa zolingalira zanu za mtengo wace ndithu! Mawerengedwe ace ndi ambirimbiri!

18 Ndikaziwerenga zicuruka koposa mcenga: Ndikauka ndikhalanso nanu.

19 Indedi, mudzaomba woipa, Mulungu: Ndipo amuna inu nkhumba mwazi, cokani kwa ine.

20 Popeza anena za Inu moipa, Ndi adani anu achula dzina lanu mwacabe.

21 Kodi sindidana nao iwo akudana ndi Inu, Yehova? Ndipo kodi sindimva nao cisoni iwo akuukira Inu?

22 Ndidana nao ndi udani weni weni: Ndiwayesa adani.

23 Mundisanthule, Mulungu, nimudziwe mtima wanga; Mundiyese nimudziwe zolingalira zanga.

24 Ndipo mupenye ngati ndiri nao mayendedwe oipa, Nimunditsogolere pa njira yosatha.

140

1 Ndilanditseni, Yehova, kwa munthu woipa; Ndisungeni kwa munthu waciwawa;

2 Amene adzipanga zoipa mumtima mwao; Masiku onse amemeza nkhondo.

3 Anola lilime lao ngati njoka; Pansi pa milomo yao pali ululu wa mphiri.

4 Ndilindireni Yehova, ndisalowe m'manja mwa woipa; Ndisungeni kwa munthu waciwawa; Kwa iwo akuti akankhe mapazi anga.

5 Odzikuzaanandichera msampha, nandibisira zingwe; Anacha ukonde m'mphepete mwa njira; Anandichera makwekwe.

6 Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga; Mundicherere khutu mau a kupemba kwanga, Yehova.

7 Yehova Ambuye, ndinu mphamvu ya cipulumutso canga, Munandiphimba mutu wanga tsiku lakulimbana nkhondo.

8 Yehova, musampatse woipa zokhumba iye; Musamthandize zodzipanga zace; angadzikuze.

9 Kunena za mutu wao wa iwo akundizinga, Coipa ca milomo yao ciwaphimbe.

10 Makala amoto awagwere; Aponyedwe kumoto; M'maenje ozama, kuti asaukenso.

11 Munthu wamlomo sadzakhazikika pa dziko lapansi; Coipa cidzamsaka munthu waciwawa kuti cimgwetse.

12 Ndidziwa kuti Yehova adzanenera wozunzika mlandu, Ndi kuweruzira aumphawi,

13 Indedi, olungama adzayamika dzina lanu; Oongoka mtima adzakhala pamaso panu,

141

1 Yehova, ndaitana kwa Inu; ndifulumireni ine; Mundicherere khutu, pamene ndiitana kwa Inu.

2 Pempherolanga liikike ngaticofukiza pamaso panu; Kukweza manja anga kuikike ngati nsembe ya madzulo.

3 Muike mdindo pakamwa panga, Yehova; Sungani pakhomo pa milomo yanga.

4 Mtima wanga usalinge ku cinthu coipa, Kucita nchito zoipa Ndi anthu akucita zopanda pace; Ndipo ndisadye zankhuli zao.

5 Akandipanda munthu wolungama ndidzati ncifundo: Akandidzudzula, ndidzakuyesa mafuta a pamutu; Mutu wanga usakane: Pakuti pangakhale posautsidwa iwo ndidzawapempherera.

6 Oweruza ao anagwetseka pambali pa thanthwe; Nadzamva mau anga kuti ndiwo okondweretsa.

7 Mafupa athu amwazika pakamwa pa manda, Monga ngati akumba nanyimphula nthaka yapansi.

8 Pakuti maso anga apenya kwanu, Yehova Ambuye; Ndithawira kwa Inu; musataye moyowanga.

9 Mundisunge ndisagwe mumsampha anandicherawo, Ndisakodwe m'makwekwe a iwo ocita zopanda pace,

10 Oipa agwe pamodzi m'maukonde ao, Kufikira nditapitirira ine.

142

1 Ndipfuula nalo liu langa kwa Yehova; Ndi mau anga ndipemba kwa Yehova.

2 Nditsanulirakudandaulakwanga pamaso pace; Ndionetsa msauko wanga pamaso pace.

3 Pamene mzimu wanga unakomoka m'kati mwanga, munadziwa njira yanga. M'njira ndiyendamo anandichera msampha,

4 Penyani ku dzanja lamanja ndipo muone; palibe wondidziwa; Pothawirapo pandisowa; palibe mmodzi wosamalira moyo wanga.

5 Ndinapfuulira kwa inu, Yehova; Ndina, Inu ndinu pothawirapo panga, Gawo langa m'dziko la amoyo.

6 Tamverani kupfuula kwanga; papeza ndisauka kwambiri; Ndilanditseni kwa iwo akundilondola; popeza andilaka.

7 Turutsani moyo wanga m'ndende, kuti ndiyamike dzina lanu; Olungama adzandizinga; Pakuti mudzandicitira zokoma.

143

1 Imvani pemphero langa, Yehova; ndicherere khutu kupemba kwanga; Ndiyankheni mwa cikhulupiriko canu, mwa cilungamo canu.

2 Ndipo musaitane mlandu wa mtumiki wanu; Pakuti pamaso panu sipadzakhala wolungama wamoyo mmodzi yense.

3 Pakuti mdani alondola moyo wanga; Apondereza pansr moyo wanga; Andikhalitsa mumdima monga iwo adafa kale lomwe.

4 Potero mzimu wanga wakomoka mwa ine; Mtima wanga utenga nkhawa m'kati mwanga,

5 Ndikumbukila masiku a kale lomwe; Zija mudazicita ndilingirirapo; Ndikamba pa ndekha za nchito ya manja anu.

6 Nditambalitsira manja anga kwa Inu: Moyo wanga ulira Inu monga dziko lolira mvula.

7 Fulumirani ndiyankheni, Yehova; mzimu wanga ukutha. Musandibisire nkhope yanu; Ndingafanane nao akutsikira kudzenje.

8 Mundimvetse cifundo canu mamawa; Popeza ndikhulupirira Inu: Mundidziwitse njira ndiyendemo; Popeza ndikweza moyo wanga kwa Inu.

9 Mundilanditse kwa adani anga, Yehova; Ndibisala mwa Inu.

10 Mundiphunzitse cokonda Inu; popeza Inu ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu ndi wokoma; munditsogolere kucidikha.

11 Mundipatse moyo, Yehova, cifukwa ca dzina lanu; Mwa cilungamo canu muturutse moyo wanga m'nsautso.

12 Ndipo mwa cifundo canu mundidulire adani anga, Ndipo muononge onse akusautsa moyo wanga; Pakuti ine ndine mtumiki wanu.

144

1 Wolemekezeka Yehova thanthwe langa, Wakuphunzitsa manja anga acite nkhondo, Zala zanga zigwirane nao:

2 Ndiye cifundo canga, ndi linga langa, Msanje wanga, ndi mpulumutsi wanga; Cikopa canga, ndi Iye amene ndimtama; Amene andigonjetsera anthu anga.

3 Yehova, munthu ndani kuti mumdziwa? Mwana wa munthu kuti mumsamalira?

4 Munthu akunga mpweya; Masiku ace akunga mthunzi wopitirira.

5 Weramutsani thambo lanu, Yehova, nimutsike: Khudzani mapiri ndipo adzafuka.

6 Ng'animitsani mphezi, ndi kuwabalalitsa; Tumizani mibvi yanu, ndi kuwapitikitsa,

7 Turutsani manja anu kucokera m'mwamba; Ndikwatuleni ndi kundilanditsa ku madzi akuru, Ku dzanja la alendo;

8 Amene pakamwa pao alankhula zacabe, Ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lacinyengo.

9 Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano, Mulungu; Pa cisakasa ca zingwe khumi ndidzayimbira zakukulemekezani.

10 Ndiye amene apatsa mafumu cipulumutso: Amene alanditsa Davide mtumiki wace ku lupanga loipa.

11 Ndilanditseni ndi kundipulumutsa ku dzanja la alendo, Amene pakamwa pao alankhula zacabe, Ndi dzanja lao lamanja ndilo dzanja lacinyengo.

12 Kuti ana athu amuna akhale ngati mmera udakula usanakhwime; Ana athu akazi ngati nsanamira za kungondya, zosema zikometsere nyumba ya mfumu.

13 Kuti nkhokwe zathu zidzale, kutipatsa za mitundu mitundu; Ndi kuti nkhosa zathu ziswane zikwi zikwi, inde zikwi khumi kubusako.

14 Kuti ng'ombe zathu zikhale zasenza katundu; Ndi kuti pasakhale kupasula linga kapena kuturukamo, Pasakhalenso kupfuula m'makwalala athu.

15 Odala anthu akuona zotere; Odala anthu amene Mulungu wao ndi Yehova.

145

1 Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu; Ndipo ndidzalemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

2 Masiku onse ndidzakuyamikani; Ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

3 Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukuru; Ndi ukulu wace ngwosasanthulika.

4 Mbadwo wina udzalemekezera nchito zanu mbadwo unzace, Ndipo udzalalikira zamphamvu zanu.

5 Ndidzalingalira ulemerero waukuru wa ulemu wanu, Ndi nchito zanu zodabwiza.

6 Ndipo adzanenera mphamvu za nchito zanu zoopsa; Ndi ukulu wanu ndidzaufotokozera.

7 Adzabukitsa cikumbukilo ca ubwino wanu waukuru, Nadzayimbira cilungamo canu.

8 Yehova ndiye wacisomo, ndi wacifundo; Osakwiya msanga, ndi wa cifundo cacikuru.

9 Yehova acitira cokoma onse; Ndi nsoni zokoma zace zigwera nchito zace zonse.

10 Nchito zanu zonse zidzakuyamikani, Yehova; Ndi okondedwa anu adzakulemekezani.

11 Adzanenera ulemerero wa ufumu wanu, Adzalankhulira mphamvu yanu;

12 Kudziwitsa ana a anthu zamphamvu zace, Ndi ulemerero waukuru wa ufumu wace.

13 Ufumu wanu ndiwo ufumu womka muyaya, Ndi kuweruza kwanu kufikira mibadwo yonse yonse.

14 Yehova agwiriziza onse akugwa, Naongoletsa onse owerama.

15 Maso a onse ayembekeza Inu; Ndipo muwapatsa cakudya cao m'nyengo zao.

16 Muniowetsa dzanja lanu, Nimukwaniritsira zamoyo zonse cokhumba cao.

17 Yehova ali wolungama m'njira zace zonse, Ndi wacifundo m'nchito zace zonse.

18 Yehova ali pafupi ndi onse akuitanira kwa Iye, Onse akuitanira kwa Iye m'coonadi.

19 Adzacita cokhumba iwo akumuopa; Nadzamva kupfuula kwao, nadzawapulumutsa.

20 Yehova asunga onse akukondana naye; Koma oipa onse adzawaononga.

21 Pakamwa panga padzanena cilemekezo ca Yehova; Ndi zinthu zonse zilemekeze dzina lace loyera ku nthawi za nthawi.

146

1 Haleluya; Ulemekeze Yehova, moyo wanga,

2 Ndidzalemekeza Yehovam'moyo mwanga; Ndidzayimbira zomlemekeza Mulungu wanga pokhala ndi moyo ine.

3 Musamakhulupirira zinduna, Kapena mwana wa munthu, amene mulibe cipulumutso mwa iye.

4 Mpweya wace ucoka, abwerera kumka ku nthaka yace; Tsiku lomwelo zotsimikiza mtima zace zitayika.

5 Wodala munthu amene akhala naye Mulungu wa Yakobo kuti amthandize, Ciyembekezo cace ciri pa Yehova, Mulungu wace;

6 Amene analenga zakumwamba ndi dziko lapansi, Nyanja ndi zonse ziri m'mwemo; Ndiye wakusunga coonadi kosatha:

7 Ndiye wakucitira ciweruzo osautsika; Ndiye wakupatsa anjala cakudya; Yehova amasula akaidi;

8 Yehova apenyetsa osaona; Yehova aongoletsa onse owerama; Yehova akonda olungama;

9 Yehova asunga alendo; Agwiriziza mwana wamasiye mkazi wamasiye; Koma akhotetsa njira ya oipa.

10 Yehova adzacita ufumu kosatha, Mulungu wako, Ziyoni, ku mibadwo mibadwo. Haleluya.

147

1 Haleluya; Pakuti kuyimbira zomlemekeza Mulungu wathu nkokoma; Pakuti cikondwetsa ici, cilemekezo ciyenera.

2 Yehova amanga Yerusalemu; Asokolotsa otayika a Israyeli.

3 Aciritsa osweka mtima, Namanga mabala ao.

4 Awerenga nyenyezi momwe ziri; Azicha maina zonsezi.

5 Ambuye wathu ndi wamkuru ndi wa mphamvu zambiri; Nzeru yace njosatha.

6 Yehova agwiriziza ofatsa; Atsitsira oipa pansi.

7 Yamikani Yehova ndi kuthira mang'ombe; Myimbireni Mulungu wathu zamlemekeza pazeze:

8 Amene aphimba thambo ndi mitambo, Amene akonzera mvula nthaka, Amene aphukitsa msipu pamapiri.

9 Amene apatsa zoweta cakudya cao, Ana a khungubwi alikulira.

10 Mphamvu ya kavalo siimkonda: Sakondwera nayo miyendo ya munthu.

11 Yehova akondwera nao akumuopa Iye, Iwo akuyembekeza cifundo cace.

12 Yerusalemu, lemekezani Yehova; Ziyoni, lemekezani Mulungu wanu.

13 Popeza analimbitsa mipiringidzo ya zitseko zanu: Anadalitsa ana anu m'kati mwanu.

14 Ndiyeamene akhalitsamalireanu mumtendere; Akukhutitsani ndi tirigu wakuca bwino.

15 Atumiza lamulo lace ku dziko lapansi; Mau ace athamanga liwiro.

16 Apatsa cipale cofewa ngati ubweya; Awaza cisanu ngati phulusa.

17 Aponya matalala ace ngati zidutsu: Adzaima ndani pa kuzizira kwace?

18 Atumiza mau ace nazisungunula; Aombetsa mphepo yace, ayenda madzi ace.

19 Aonetsa mau ace kwa Yakobo; Malemba ace, ndi maweruzo ace kwa Israyeli.

20 Sanatero nao anthu amtundu wina; Ndipo za maweruzo ace, sanawadziwa. Haleluya.

148

1 Haleluya. Lemekezani Yehova kocokera kumwamba; Mlemekezeni m'misanje.

2 Mlemekezeni, angelo ace onse; Mlemekezeni, makamu ace onse.

3 Mlemekezeni, dzuwa ndi mwezi; Mlemekezeni, nyenyezi zonse zaunikira.

4 Mlemekezeni, m'mwambamwamba, Ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo.

5 Alemekeze dzina la Yehova; Popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.

6 Anazikhazikanso ku nthawi za nthawi; Anazipatsa cilamulo cosatumphika.

7 Lemekezani Yehova kocokera ku dziko lapansi, Zinsomba inu, ndi malo ozama onse;

8 Moto ndi matalala, cipale cofewa ndi nkhungu; Mphepo ya namondwe, yakucita mau ace;

9 Mapiri ndi zitunda zonse; Mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse:

10 Nyama za kuthengo ndi zoweta zonse; Zokwawa, ndi mbalame zakuuluka;

11 Mafumu a padziko ndi mitundu yonse ya anthu; Zinduna ndi oweruza onse a padziko;

12 Anyamata ndiponso anamwali; Okalamba pamodzi ndi ana:

13 Alemekeze dzina la Yehova; Pakuti dzina lace lokha ndi lokwezeka; Ulemerero wace uli pamwamba pa dziko lapansi ndi thambo.

14 Ndipo anakweza nyanga ya anthu ace, Cilemekezo ca okondedwa ace onse; Ndiwo ana a Israyeli, anthu a pafupi pa Iye, Haleluya,

149

1 Haleluya, Myimbireni Yehova nyimbo yatsopano, Ndi cilemekezo cace mu msonkhano wa okondedwa ace.

2 Akondwere Israyeli mwa Iye amene anamlenga; Ana a Ziyoni asekere mwa Mfumu yao.

3 Alemekeze dzina lace ndi kuthira mang'ombe; Amyimbire zomlemekeza ndi lingaka ndi zeze.

4 Popeza Yehova akondwera nao anthu ace; Adzakometsa ofatsa ndi cipulumutso,

5 Okondedwa ace atumphe mokondwera m'ulemu: Apfuule mokondwera pamakama pao,

6 Nyimbo zakukweza Mulungu zikhale pakamwa pao, Ndi lupanga lakuthwa konse konse m'dzanja lao;

7 Kubwezera cilango akunja, Ndi kulanga mitundu ya anthu;

8 Kumanga mafumu ao ndi maunyolo, Ndi omveka ao ndi majerejede acitsulo;

9 Kuwacitira ciweruzo colembedwaco: Ulemu wa okondedwa ace onse ndi uwu. Haleluya.

150

1 Haleluya, Lemekezani Mulungu m'malo ace oyera; Mlemekezeni m'thambo la mphamvu yace.

2 Mlemekezeni cifukwa ca nchito zace zolimba; Mlemekezeni monga mwa ukulu wace waunjinji.

3 Mlemekezeni ndi kulira kwa lipenga; Mlemekezeni ndi cisakasa ndi zeze.

4 Mlemekezeni ndi lingaka ndi kuthira mang'ombe: Mlemekezeni ndi zoyimbira za zingwe ndi citoliro.

5 Mlemekezeni ndi nsanje zomveka: Mlemekezeni ndi nsanje zoliritsa.

6 Zonse zakupuma zilemekeze Yehova. Haleluya.