1 PAULO, mtumwi wa Kristu Yesu, mwa cifuniro ca Mulungu, ndi Timoteo mbaleyo, kwa Mpingo wa Mulungu umene uli ku Korinto, pamodzi ndi oyera mtima onse amene ali m'Akaya lonse:
2 Cisomo kwa inu ndi mtendere zocokera kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Kristu.
3 Wolemekezeka Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Kristu, Atate wa zifundo ndi Mulungu wa citonthozo conse,
4 woo titonthoza ife m'nsautso yathu yonse, kuti tidzathe ife kutonthoza iwo okhala m'nsautso iri yonse, mwa citonthozo cimene titonthozedwa naco tokha ndi Mulungu.
5 Pakuti monga masautso a Kristu aticurukira ife, coteronso citonthozo cathu cicuruka mwa Kristu,
6 Koma ngati tisautsidwa, kuli cifukwa ca citonthozo ndi cipulumutso canu; ngati titonthozedwa, kuli kwa citonthozo canu cimene cicititsa mwa kupirira kwa masautso omwewo amene ifenso timva.
7 Ndipo ciyembekezo cathu ca kwa inu ncokbazikika; podziwa kuti monga muli oyanjana ndi masautsowo, koteronso ndi citonthozo.
8 Pakuti sitifuna abale, kuti mukhale osadziwa za cisautso cathu tinakomana naco m'Asiya, kuti tinathodwa kwakukuru, koposa mphamvu yathu, kotero kuti tinada nkhawa ngakhale za moyo wathu;
9 koma tokha tinakhala naco citsutso ca imfa mwa ife tokha, kuti tisalimbike pa ife tokha, koma pa Mulungu wakuukitsa akufa;
10 amene anatilanditsa mu imfa yaikuru yotere, nadzalanditsa;
11 amene timyembekezera kuti adzalanditsanso; pothandizana inunso ndi pemphero lanu la kwa ife; kuti pa mphatso ya kwa ife yodzera kwa anthu ambiri, payamikike ndi anthu ambiri cifukwa ca ife.
12 Pakuti kudzitamandira kwathu ndiko umboni wa cikumbu mtima cathu, kuti m'ciyero ndi kuona mtima kwa Mulungu, si m'nzeru ya thupi, koma m'cisomo ca Mulungu tinadzisunga m'dziko lapansi, koma koposa kwa inu.
13 Pakuti sitilemba kwa inu zina, koma zimene muwerenga, kapenanso mubvomereza; ndipo ndiyembekeza kuti mudzabvomereza kufikira cimariziro;
14 monganso munatibvomerezera ife pena, kuti ife ndife kudzitamandira kwanu, monga momwe inunso muli kudzitamandira kwathu m'tsiku la Ambuye wathu Yesu.
15 Ndipo m'kulimbika kumene ndinafuna kudza kwa inu kale, kuti mukakhalenaco cisomo caciwiri;
16 ndipo popyola kwanu kupita ku Makedoniya, ndi kudzanso kwa inu pobwera kufuma ku Makedoniya; ndi kuperekezedwa ndi inu ku Yudeya.
17 Pamenepo, pakufuna cimene, kodi ndinacitapo kosinthasintha? Kapena zimene nditsimikiza mtima kodi ndizitsimikiza mtima monga mwa thupi? Kuti pa ine pakhale eya, eya, ndi iai, iai?
18 Koma Mulungu ali wokhulupirika, kuti mau athu a kwa inu sanakhala eya ndi iai.
19 Pakuti Mwana wa Mulungu, Yesu Kristu, amene analalikidwa mwa inu ndi ife, (ine ndi Silvano ndi Timoteo) sanakhala eya ndi iai, koma anakhala eya mwa iye.
20 Pakuti monga mawerengedwe a malonjezano a Mulungu ali mwa iye eya; cifukwa cacenso ali mwa iye Amen, kwa ulemerero wa Mulungu mwa ife.
21 Koma iye wakutikhazika pamodzi ndi inu kwa Kristu, natidzoza ife, ndiye Mulungu;
22 amenenso anatisindikiza cizindikilo, natipatsa cikole ca Mzimu mu mitima yathu.
23 Koma ine ndiitana Mulungu akhale mboni pa moyo wanga, kud kulekera inu ndinaleka kudza ku Korinto.
24 Si kuti ticita ufumu pa cikhulupiriro canu, koma tikhala othandizana naco cimwemwe canu; pakuti ndi cikhulupiriro muimadi.
1 Koma ndinatsimikiza mtima mwa ine ndekha, ndisadzenso kwa inu ndi cisoni.
2 Pakuti ngati ine ndimvetsa inu cisoni, ndaninso amene adzandikondweretsa ine, kama iye amene ndammvetsa cisoni?
3 Ndipo ndinalemba ici comwe, kuti pakudza ndisakhale naco cisoni kwa iwo amene ayenera kukondweretsa ine; ndi kukhulupirira mwa inu nonse, kuti cimwemwe canga ndi canu ca inu nonse.
4 Pakuti m'cisautso cambiri ndi kuwawa mtima ndinalembera inu ndi misozi yambiri; si kuti ndikumvetseni cisoni, koma kuti mukadziwe cikondi ca kwa inu, cimene ndiri naco koposa.
5 Koma ngati wina wacititsa cisoni, sanacititsa cisoni ine, koma pena (kuti ndisasenzetse) inu nonse.
6 Kwa wotereyo cilango ici cidacitika ndi ambiri cikwanira;
7 kotero kwina kuti inu mumkhululukire ndi kumtonthoza, kuti wotereyo mgamizidwe ndi cisoni cocurukaco.
8 Cifukwa cace ndikupemphani inu kuti mumtsimikizire ameneyo cikondi canu.
9 Pakuti cifukwa ca ici ndalembanso, kuti ndidziwe mayesedwe anu, ngati muli omvera m'zonse.
10 Koma amene mumkhululukira kanthu, inenso nditero naye; pakuti cimene ndakhululukira inenso, ngati ndakhululukira kanthu, ndacicita cifukwa ca inu, pamasopa Kristu;
11 kuti asaticenierere Satana; pakuti sitikhala osadziwa macenjerero ace.
12 Koma pamene ndinadza ku Trowa kudzalalikira Uthenga Wabwino wa Kristu, ndipo pamene padanditsegukira kwa ine pakhomo, mwa Ambuye,
13 ndinalibe mpumulo mu mzimu wanga, posapeza ine Tito mbale wanga; koma polawirana nao ndinanka ku Makedoniya.
14 Koma ayamikike Mulungu, amene atitsogolera m'cigonjetso mwa Kristu, namveketsa pfungo la cidziwitso cace mwa ife pamalo ponse.
15 Pakuti ife ndife pfungo labwino la Kristu, kwa Mulungu, mwa iwo akupulumutsidwa, ndi mwa iwo akuonongeka; kwa ena pfungo la imfa kuimfa;
16 koma kwa ena pfungo la moyo kumoyo. Ndipo azikwanira ndani izi?
17 Pakuti sitikhala monga ambiriwo, akucita malonda nao mau a Mulungu; koma monga mwa coona mtima, koma monga mwa Mulungu pamaso pa Mulungu, tilankhula mwa Kristu.
1 Kodi tirikuyambanso kudzibvomereza tokha? kapena kodi tisowa, monga ena, akalata otibvomerezetsa kwa inu, kapena ocokera kwa inu?
2 Inu ndinu kalata wathu, wolembedwa mu mitima yathu, wodziwika ndi wowerengedwa ndi anthu onse;
3 popeza mwaonetsedwa kuti muli kalata wa Kristu, wakumtumikira ndi ife, wosalembedwa ndi kapezi iai, koma ndi Mzimu wa Mulungu wamoyo; wosatim'magome amiyala, koma m'magome a mitima yathupi.
4 Ndipo kulimbika kotere kwa Mulungu tiri nako mwa Kristu:
5 si kuti tiri okwanira pa ife tokha, kuyesera kanthu monga mocokera mwa ife tokha; kukwanira kwathu kucokera kwa Mulungu;
6 amenenso anatikwaniritsa ife tikhale atumiki a pangano latsopano; si la cilembo, koma la mzimu; pakuti cilembo cipha, koma mzimu ucititsa moyo.
7 Komangati utumiki wa imfa wolembedwa ndi wolocedwa m'miyala, unakhala m'ulemerero, kotero kuti ana a Israyeli sanathe kuyang'anitsa pankhope yace ya Mose, cifukwa ca ulemerero wa nkhope yace, umene unalikucotsedwa:
8 koposa kotani nanga utumiki wa Mzimu udzakhala m'ulemerero?
9 Pakuti ngati utumiki wa citsutso unali wa ulemerero, makamaka utumiki wa cilungamo ucurukira muulemerero kwambiri.
10 Pakutinso cimene cinacitidwa ca ulemerero sicinacitidwa ca ulemerero m'menemo, cifukwa ca ulemerero woposawo.
11 Pakuti ngati cimene cirikucotsedwa cinakhala m'ulemerero, makamaka kwambiri cotsalaco ciri m'ulemerero.
12 Pokhala naco tsono ciyembekezo cotere, tilankhula ndi kukhazikika mtima kwakukuru,
13 ndipo si monga Mose, amene anaika cophimba pa nkhope yace, kuti ana a lsrayeli asayang'anitse pa cimariziro ca cimene cinalikucotsedwa;
14 koma mitima yao inaumitsidwa; pakuti kufikira lero lomwe lino, pa lcuwerenga kwa pangano lakale cophimba comweci cikhalabe cosabvundukuka, cimene cirikucotsedwa mwa Kristu.
15 Koma kufikira lero, pamene awerengedwa Mose, cophimba cigona pamtima pao.
16 Koma pamene akatembenukira kwa Mulungu, cophimbaco cieotsedwa.
17 Koma Ambuye ndiye Mzimuyo; ndipo pamene pali Mzimu wa Ambuye pali ufulu.
18 Koma ife tonse ndi nkhope yosaphimbika popenyerera monga mwa kalirole ulemerero wa Ambuye, tisandulika m'cithunzihunzi comweci kucokera kuulenerero kumka kuulemerero, monga ngati kucokera kwa Ambuye Mzimu.
1 Cifukwa cace popeza tiri nao utumiki umene, monga talandira cifundo, sitifoka;
2 koma takaniza zobisfka za manyazi, osayendayenda mocenjerera, kapena kucita nao mau a Mulungu konyenga; koma ndi maonekedwe a coonadi tidzibvomeretsa tokha ku cikumbu mtima ca anthu onse pamaso pa Mulungu.
3 Koma ngatinso Uthenga Wabwino wathu uphimbika, uphimbika mwa iwo akutayika;
4 mwa amene mulungu wa nthawi yino ya pansi pano unacititsa khungu maganizo ao a osakhulupirira, kuti ciwalitsiro ca Uthenga Wabwino wa ulemerero wa Kristu, amene ali cithunzithunzi ca Mulungu, cisawawalire.
5 Pakuti tilalikira si za ife tokha, koma Kristu Yesu Ambuye, ndi ife tokha akapolo anu, cifukwa ca Kristu.
6 Pakuti Mulungu amene anati, Kuunika kudzawala kuturuka mumdima, ndiye amene anawala m'mitima yathu kutipatsa ciwalitsiro ca cidziwitso ca ulemerero wa Mulungu pankhope pa Yesu Kristu.
7 Koma tiri naco cuma ici m'zotengera zadothi, kuti ukulu woposa wamphamvu ukhale wa Mulungu, wosacokera kwa ife;
8 ndife osautsika monsemo, koma osapsinjika; osinkhasinkha, koma osakhala kakasi;
9 olondoleka, koma osatayika; ogwetsedwa, koma osaonongeka;
10 nthawi zonse tirikusenzasenza m'thupi kufa kwace kwa Yesu, kuti moyonso wa Yesu uoneke m'thupi mwathu.
11 Pakuti ife amene tiri ndi moyo tiperekeka kuimfa nthawi zonse, cifukwa ca Yesu, kuti moyonso wa Yesu uoneke m'thupi lathu lakufa.
12 Cotero imfa icita mwa ife, koma moyo mwa inu.
13 Koma pokhala nao mzimu womwewo wa cikhulupiriro, monga mwa colembedwaco, ndinakhulupira, cifukwa cace ndinalankhula; ifenso tikhulupira, cifukwa cace tilankhula;
14 podziwa kuti iye amene anaukitsa Ambuye Yesu adzaukitsa ifenso pamodzi ndi Yesu, nadzatiikapo pamodzi ndi inu.
15 Pakuti zonsezi nza kwa inu, kuti cisomoco, cocurukitsidwa mwa unyinjiwo, cicurukitsire ciyamiko ku ulemerero wa Mulungu.
16 Cifukwa cace sitifoka; koma ungakhale umunthu wathu wakunja ubvunda, wa m'kati mwathu ukonzedwa kwatsopano tsiku ndi tsiku.
17 Pakuti cisautso cathu copepuka ca kanthawi citicitira ife kulemera koposa kwakukuru ndi kosatha kwa ulemerero;
18 popeza sitipenyerera zinthu zooneka, koma zinthu zosaoneka; pakuti zinthu zooneka ziri za nthawi, koma zinthu zosaoneka ziri zosatha.
1 Pakuti tidziwa kuti ngati nyumba ya pansi pano ya msasa wathu ipasuka, tiri naco cimango ca kwa Mulungu, ndiyo nyumba yosamangidwa ndi manja, yosatha, m'Mwamba.
2 Pakutinso m'menemo tibuula, ndi kukhumbitsa kubvekedwa ndi cokhalamo cathu cocokera Kumwamba;
3 ngatitu pobvekedwa sitidzapezedwa amarisece.
4 Pakutinso ife okhala mu msasawu tibuula, pothodwa; si kunena kuti tifuna kubvulidwa, koma kubvekedwa, kuti caimfaco cimezedwe ndi moyo.
5 Ndipo wotikonzera ife ici cimene, ndiye Mulungu, amene anatipatsa ife cikhole ca Mzimu,
6 Pokhala nako kulimbika mtima nthawi zonse tsono, ndipo podziwa kuti pamene tiri kwathu m'thupi, sitiri kwa Ambuye,
7 (pakuti tiyendayenda mwa cikhulupiriro si mwa cionekedwe);
8 koma tilimbika mtima, ndipo tikondwera makamaka kusakhala m'thupi, ndi kukhala kwathu kwa Ambuye.
9 Cifukwa cacenso tifunitsitsa, kapena kwathu kapena kwina, kukhala akumkondweretsa iye.
10 Pakuti ife tonse tiyenera kuonetsedwa ku mpando wa kuweruza wa Kristu, kuti yense alandire zocitika m'thupi, monga momwe anacita, kapena cabwino kapena coipa.
11 Podziwa tsono kuopsa kwa Ambuye, tikopa anthu, koma tionetsedwa kwa Mulungu; ndipo ndiyembekezanso kuti tionetsedwa m'zikumbu mtimazanu.
12 Sitidzibvomeretsanso ife tokha kwa inu, koma tikupatsani inu cifukwa ca kudzitamandira pa ife, kuti mukakhale nako kanthu kakutsutsana nao iwo akudzitamandira pooneka pokha, osati mumtima.
13 Pakuti ngati tiri oyaruka, titero kwa Mulungu; ngati tiri a nzeru zathu, titero kwa inu.
14 Pakuti cikondi ca Kristu citikakamiza; popeza taweruza cotero, kuti mmodzi adafera onse, cifukwa cace onse adafa;
15 ndipo adafera onse, kuti iwo akukhala ndi moyoasakhalenso ndi moyo kwa iwo okha, koma kwa iye amene adawafera iwo, nauka.
16 Kotero kuti ife sitidziwanso munthu tsopano monga mwa thupi; ndipo ngati tazindikira Kristu monga mwa thupi, koma tsopano sitimzindikiranso motero.
17 Cifukwa cace ngati munthu ali yense ali mwa Kristu ali wolengedwa watsopano; zinthu zakale zapita, taonani, zakhala zatsopano,
18 Koma zinthu zonse zicokera kwa Mulungu amene anatiyanjanitsa kwa iye yekha mwa Kristu, natipatsa utumiki wa ciyanjanitso;
19 ndiko kunena kuti Mulungu anali mwa Kristu, alinkuyanjanitsa dziko lapansi kwa Iyeyekha, osawawerengera zolakwa zao; ndipo anaikiza kwa ife mau a ciyanjanitso,
20 Cifukwa cace tiri atumiki m'malo mwa Kristu, monga ngati Mulungu alikudandaulira mwa ife; tiumiriza inu m'malo mwa Kristu, yanjanitsidwani ndi Mulungu,
21 Ameneyo sanadziwa ucimo anamyesera ucimo m'malo mwathu; kuti ife tikhale cilungamo ca Mulungu mwa iye.
1 Ndipo a ocita naye pamodzi tidandauliranso kuti musalandire cisomo ca Mulungu kwacabe inu,
2 (pakuti anena, M'nyengo yolandiridwa ndinamva iwe, Ndipo m'tsiku la cipulumutso ndinakuthandiza; Taonani, tsopano ndiyo nyengo yabwino yolandiridwa, taonani, tsopano ndilo tsiku la cipulumutso);
3 osapatsa cokhumudwitsa konse m'cinthu ciri conse, kuti utumikiwo usanenezedwe;
4 koma m'zonse tidzitsimikfzira ife tokha monga atumiki a Mulungu, m'kupirira kwambiri, m'zisautso, m'zikakamizo, m'zopsinja,
5 m'mikwingwirima, m'ndende, m'mapokoso, m'mabvutitso, m'madikiro, m'masalo a cakudya;
6 m'mayeredwe, m'cidziwitso, m'cilekerero, m'kukoma mtima, mwa Mzimu Woyera, m'cikondi cosanyenga;
7 m'mau a coonadi, mu mphamvu ya Mulungu; mwa camuna ca cilungamo kulamanja ndi kulamanzere,
8 mwa ulemerero, mwa mnyozo, mwa mbiri yoipa ndi mbiri yabwino; mongaosoceretsa, angakhale ali oona;
9 monga osadziwika, angakhale adziwika bwino; monga alinkufa, ndipo taonani, tiri ndi moyo; monga olangika, ndipo osaphedwa;
10 monga akumva cisoni, koma akukondwera nthawi zonse; monga aumphawi, lroma akulemeretsa ambiri; mensa okhala opanda-kanthu, ndipo akhala nazo zinthu zonse.
11 M'kamwa mwathu mmotseguka kwa inu Akorinto, mtima wathu wakulitsidwa.
12 Simupsinjika mwa ife, koma mupsiniika mumtima mwanu.
13 Ndipo kukhale cibwezero comweci (ndinena monga ndi ana anga) mukulitsidwe inunso.
14 Musakhale omangidwa m'goli ndi osakhulupira osiyana; pakuti cilungamo cigawanabwanji ndi cosalungama? Kapena kuunika kuyanjana bwanji nw mdima?
15 Ndipo Kristu abvomerezana bwanji ndi Beliyali? Kapena wokhulupira ali nalo gawo lanji pamodzi ndi wosakhulupira?
16 Ndipo ciphatikizo cace ncanji ndi kacisi wa Mulungu ndi wa mafano? Pakuti ife ndife kacisi wa, Mulungu wamoyo; monga Mulungu anati, Ndidzakhalitsa mwa iwo, ndipe ndidzayendayenda mwa iwo; ndipo ndidzakhala Mulungu wao, ndi iwo adzakhala anthu anga.
17 Cifukwa cace, Turukani pakati Pao, ndipo patukani, ati Ambuye, Ndipo musakhudza kanthu kosakonzeka; Ndipo Ine ndidzalandira inu,
18 Ndipo ndidzakhala kwa inu Atate, Ndi inu mudzakhala kwa Ine ana amunandi akazi, anena Ambuye Wamphamvuyonse.
1 Pokhala nao tsono malonjezano amenewa, okondedwa, tidzikonzere tokha kuleka codetsa conse ca thupi ndi ca mzimu, ndi kutsirfza ciyero m'kuopa Mulungu.
2 Tipatseni malo; sitinamcitira munthu cosalungama, sitinaipsa munthu, sitinacenjerera munthu.
3 Sindinena ici kuti ndikutsutseni: pakuti ndanena kale kuti muli mu mitima yathu, kuti tife limodzi ndi kukhala ndi moyo limodzi.
4 Ndilimbika mtima kwambiri pakunena nanu, kudzitamandira kwanga cifukwa ca inu nkwakukuru; ndidzazidwa naco citonthozo, ndisefukira naco cimwemwe m'cisautso cathu conse.
5 Pakutinso pakudza ife m'Makedoniya thupi lathu linalibe mpumulo, koma tinasautsidwa ife monsemo; kunjako zolimbana, m'katimo mantha.
6 Koma iye amene atonthoza odzicepetsa, ndiye Mulungu, anatitonthoza ife ndi kufika kwace kwa Tito;
7 koma si ndi kufika kwace kokha, komanso ndi citonthozo cimene anatonthozedwa naco mwa inu, pamene anatiuza ife kukhumbitsa kwanu, kulira kwanu, cangu canu ca kwa ine; kotero kuti ndinakondwera koposa,
8 Kuti ngakhale ndakumvetsani cisoni ndi kalata uja, sindiwawapo mtima, ndingakhale ndinawawa mtima; pakuti ndiona kuti kalata uja anakumvetsani cisoni, ngakhale kwa nthawi yokha.
9 Tsopano ndikondwera, sikuti mwangomvedwa cisoni, koma kuti mwamvetsedwa cisoni ku kutembenuka mtima; pakuti munamvetsedwa cisoni ca kwa Mulungu, kuti tisakusowetseni m'kanthu kali konse.
10 Pakuti cisoni ca kwa Mulungu citembenuzira mtima kueipulumutso, cosamvetsanso cisoni; koma cisonicadziko lapansi cicita imfa.
11 Pakuti, taonani, ici comwe, cakuti mudamvetsedwa cisoni ca kwa Mulungu, khama lalikuru lanji cidalicita mwa inu, komanso codzikonza, komanso mkwiyo, komanso mantha, komanso kukhumbitsa komanso cangu, komanso kubwezera cilango! M'zonse muoadzitsimikizira nokha kuti muli oyera mtima m'menemo.
12 Cifukwa cace ndingakhale ndalembera kwa inu, sindinacita cifukwa ca iye amene anacita coipa, kapena cifukwa ca iye amene anacitidwa coipa, koma kuti khama lanu la kwa ife lionetsedwe kwa inu pamaso pa Mulungu.
13 Cifukwa ca icitatonthozedwa; ndipo m'citonthozo cathu tinakondwera koposa ndithu pa cimwemwe ca Tito, kuti mzimu wace unatsitsimutsidwa ndi inu nonse.
14 Pakuti ngati ndadzitamandira nako kanthu kwa iye cifukwa ca inu, sindinamvetsedwa manyazi; koma monga tinalankhula zonse ndi inu m'coonadi, koteronso kudzitamandira kwathu kumene kwa Tito, kunakhala coonadi.
15 Ndipo cikondi ceni ceni care cicurukira koposa kwa inu, pokumbukira kumvera kwanu kwa inu nonse, kuti munamlandira iye ndi mantha ndi kunthunthumira.
16 Ndikondwera kuti m'zonse ndilimbika mtima za inu.
1 Ndipo tikudziwitsani, abale, cisomo ca Mulungu copatsika mwa Mipingo ya ku Makedoniya,
2 kuti m'citsimikizo cacikuru ca cisautso, kucurukitsa kwa cimwemwe cao, ndi kusauka kwaokweni kweni zidacurukira ku colemera ca kuolowa mtima kwao.
3 Pakuti monga mwa mphamvu yao, ndicitapo umboni, inde koposa mphamvu yao,
4 anacita eni ace, natiumirfza ndi kutidandauliraza cisomoco, ndi za ciyanjano ca utumiki wa kwa oyera mtima;
5 ndipo, si monga tidayembekeza; koma anayamba kudzipereka okha kwa Ambuye, ndi kwa ife mwa cifuniro ca Mulungu.
6 Kotero kuti tinadandaulira Tito, kuti monga anayamba kale, comweconso atsirize kwa inu cisomo icinso.
7 Koma monga mucurukira m'zonse, m'cikhulupiriro, ndi m'mau, ndi m'cidziwitso, ndi m'khama lonse, ndi m'cikondi canu ca kwa ife, curukaninso m'cisomo ici.
8 Sindinena ici monga kulamulira, koma kuyesa mwa khama la ena coonadi ca cikondi canunso.
9 Pakuti mudziwa cisomo ca Ambuye wathu Yesu Kristu, kuti, cifukwa ca inu anakhala wosauka, angakhale anali wolemera, kuti inu ndi kusauka kwace mukakhale olemera.
10 Ndipo m'menemo odichula coyesa ine; pakuti cimene cipindulira inu, amene munayamba kale caka capitaci si kucita kokha, komanso kufunira.
11 Koma tsopano tsirizani kucitaku; kuti monga kunali cibvomerezo ca kufunira, koteronso kukhale kutsiriza kwacem'cimene muli naco.
12 Pakuti ngati cibvomerezoco ciri pomwepo, munthu alandiridwa monga momwe ali naco, si monga cimsowa.
13 Pakuti sinditero kuti ena akamasuke, ndi inu musautsidwe;
14 koma mwa kulingana kucuruka kwanu kukwanire kusowa kwao nthawi ya makono ano, kutinso kucuruka kwao kukwanire kusowa kwanu,
15 Kuti pakhalecilingano; monga kwalembedwa, Wosonkhetsacambiri sicinamtsalira; ndi iye wosonkhetsa pang'ono sicinamsowa.
16 Koma ayamikike Mulungu, wakupatsa khama lomweli la kwa inu mu mtima wa Tito.
17 Pakutitu analandira kudandaulira kwathu; koma pokhala halo khama loposa, anaturukira kunka kwil inu mwini wace.
18 Ndipo tatuma pamodzi naye mbaleyo, amene kusimba kwace m'Uthenga Wabwino kuli m'Mipingo yonse;
19 ndipo si ici cokha, komanso anasankhika ndi Mipingo, apite limodzi ndi ife m'cisomo ici, cimene ticitumikira ife, kwa ulemerero wa Ambuye, ndi kuonetsa cibvomerezo cathu;
20 ndi kupewa ici kuti wina angatichule za kucurukira kumene tikutumikira;
21 pakuti tikonzeratu zinthu zokoma, si pamaso pa Ambuye pokha, komanso pamaso pa anthu.
22 Ndipo tinatumiza mbale wathu awaperekeze iwo, amene tamtsimikizirakawiri kawiri ali wakhama m'zinthu zambiri, koma tsopano wa khama loposatu ndi kulimbika kwakukuru kumene ali nako kwa inu,
23 Nanga za Tito, ali woyanjana wanga ndi wocita nane wa kwa inu; nanga abale athu, ali atumwi a Mipingo, ali ulemerero wa Kristu.
24 Cifukwa cace muwatsimikizire iwo citsimikizo ca cikondi canu, ndi ca kudzitamandira kwathu pa inu pamaso pa Mipingo.
1 Pakutitu za utumiki wa kwa oyera mtima sikufunika kwa ine kulembera inu;
2 pakuti ndidziwa cibvomerezo canu cimene ndidzitamandira naco cifukwa ca inu ndi Amakedoniya, kuti Akaya anakonzekeratu citapita caka; ndi cangu canu cinautsa ocurukawo.
3 Koma ndatuma abale kuti kudzitamandira kwathu kwa pa inu kusakhale kopanda pace m'menemo; kuti, monga ndinanena, mukakhale okonzekeratu;
4 kuti kapena akandiperekeze a ku Makedoniya nadzakupezani inu osakonzeka, ife (kuti tisanene inu) tingacititsidwe manyazi m'kulimbika kumene.
5 Cifukwa cace ndinayesa kuti kufunika kupempha abale kuti atsogole afike kwa inu, nakonzeretu dalitso lanu lolonjezeka kale, kuti cikhale cokonzeka comweci, monga ngati mdalitso, ndipo si monga mwa kuumiriza.
6 Koma nditi ici, kuti iye wakufesa mouma manja, mouma manjanso adzatuta. Ndipo iye wakufesa moolowa manja, moolowa manjanso adzatuta.
7 Yense acite monga anatsimikiza mtima, si mwa cisoni kapena mokakamiza, pakuti Mulungu akonda wopereka mokondwerera.
8 Ndipo Mulungu akhoza kucurukitsira cisomo conse kwa inu; kuti inu, pokhala naco cikwaniro conse m'zinthu zonse, nthawi zonse, mukacurukire ku nchito yonse yabwino;
9 monga kwalembedwa; Anabalalitsa, anapatsa kwa osauka; Cilungamo cace cikhala ku nthawi yonse.
10 Ndipo iye wopatsa mbeu kwa wofesa, ndi mkate ukhale cakudya, adzapatsa ndi kucurukitsa mbeu yanu yofesa, nadzaonjezapo pa zipatso za cilungamo canu;
11 polemeretsedwa inu m'zonse ku kuolowa manja konse, kumene kucita mwa ife ciyamiko ca kwa Mulungu,
12 Pakuti utumiki wa kutumikira kumene sudzaza zosowa za oyera mtima zokha, koma ucurukiranso kwa Mulungu mwa mayamiko ambiri;
13 popeza kuti mwa kuyesa kwa utumiki umene alemekeza Mulungu pa kugonia kwa cibvomerezo canu ku Uthenga Wabwino wa Kristu, ndi kwa kuolowa manja kwa cigawano canu kwa iwo ndi kwa onse;
14 ndipo iwo, ndi pempherero lao la kwa inu, akhumbitsa inu, cifukwa ca cisomo coposa ca Mulungu pa inu,
15 Ayamikike Mulungu cifukwa ca mphatso yace yace yosatheka kuneneka.
1 Koma ine ndekha Paulo, ndidandaulira inu mwa kufatsa ndi ulere wa Kristu, ine amene pamaso panu ndikhala wodzicepetsa pakati pa inu, koma pokhala kwina ine ndilimbika mtima kwa inu;
2 koma ndipempha kuti pokhala ndiri pomwepo, ndisalimbike mtima ndi kulimbika kumene ndiyesa kulimbika nako pa ena, amene atiyesera ife monga ngati tirikuyendayenda monga mwa thupi,
3 Pakuti pakuyendayenda m'thupi, siticita nkhondo monga mwa thupi,
4 (pakuti zida za nkhondo yathu siziri za thupi, koma zamphamvu mwa Mulungu zakupasula malinga);
5 ndi kugwetsa matsutsano, ndi cokwezeka conse cimene cidzikweza pokana ddziwitso ca Mulungu, ndi kugonjetsa ganizo lonse ku kumvera kwa Kristu;
6 ndi kukhala okonzeka Irubwezera cilango kusamvera konse, pamene kumvera kwanu kudzakwaniridwa.
7 Kodi mupenyera zopenyeka pamaso? Ngati wina alimbika mwa yekha kuti ali wa Kristu, ayesere icinso mwa iye yekha, kuti monga iye ali wa Kristu, koteronso ife.
8 Pakuti ndingakhale ndikadzitamandira kanthu kocurukira za ulamuliro (umene anatipatsa Ambuye ku kumangirira, ndipo si ku kugwetsera kwanu), sindidzanyazitsidwa;
9 kuti ndisaoneke monga ngati kukuopsani mwa akalatawo.
10 Pakuti, akalatatu, ati, ndiwo olemera, ndi amphamvu; koma maonekedwe a thupi lace ngofoka, ndi mau ace ngacabe.
11 Wotereyo ayese ici kuti monga tiri ife ndi mau mwa akalata, pokhala palibe ife, tiri oterenso m'macitidwe pokhala tiri pomwepo.
12 Pakuti sitilimba mtima kudziwerenga, kapena kudzilinganiza tokha ndi ena a iwo amene adzibvomeretsa okha; koma iwowa, podziyesera okha ndi iwo okha, ndi kudzilinganiza okha ndi iwookha, alibe nzeru.
13 Koma ife sitidzadzitamandira popitirira muyeso, koma monga mwa muyeso wa cilekelezero cimene Mulungu anatigawira muyeso, kufikira ngakhale kwa inunso.
14 Pakuti sitinyanyampiradi tokha, monga ngati sitinafikira kwa inu; pakuti tinadza kufikira inunso, mu Uthenga Wabwino wa Kristu:
15 osadzitamandira popitirira muyeso mwa macititso a ena; koma tiri naco ciyembekezo kuti pakukula cikhulupiriro canu, tidzakulitsidwa mwa inu monga mwa cilekezero cathu kwa kucurukira,
16 kukalalikira Uthenga Wabwino m'tsogolo mwace mwa inu, sikudzitamandira mwa cilekezero ca wina, ndi zinthu zokonzeka kale.
17 Koma iye wodzitamandira adzitamandire mwa Ambuye;
18 pakuti si iye amene adzitama yekha, koma iye amene Ambuye amtama ali wobvomerezeka.
1 Mwenzi mutandilola pang'ono ndi copusaco! Komanso mundilole.
2 Pakuti ndicita nsanje pa inu ndi nsanje ya Mulungu; pakuti ndinakupalitsani ubwenzi mwamuna mmodzi, kuti ndikalangize inu ngati namwali woyera mtima kwa Kristu.
3 Koma ndiopa, kuti pena, monga njoka inanyenga Heva ndi kucenjerera kwace, maganizo anu angaipsidwe kusiyana nako kuona mtima ndi kuyera mtima ziri kwa Kristu.
4 Pakutitu ngati iye wakudza alalikira Yesu wina, amene ife sitinalalikira, kapena ngati mulandira mzimu wa mtundu wina, umene simunalandira, kapena uthenga wabwino wa mtundu wina umene simunalandira, mulolana nave bwino lomwe.
5 Pakuti ndiyesa kuti sindinaperewera konse ndi atumwi oposatu,
6 Ndipo ndingakhale ndiri wosaphunzira m'manenedwe, koma sinditero m'cidziwitso, koma m'zonse tacionetsa kwa inu mwa anthu onse.
7 Kodi ndacimwa podzicepetsa ndekha, kuti inu mukakwezedwe, popeza ndinalalikira kwa inu Uthenga Wabwino wa Mulungu mwaufulu?
8 ndinalanda za Mipingo yina, ndi kulandira kwa iwo kulipira kuti ndikatumikire inu;
9 ndipo pakukhala nanu, ndi kusowa, sindinasaukitsa munthu ali yense; pakuti abale akucokera ku Makedoniya, anakwaniritsa kusowa kwanga; ndipo m'zonse ndinacenjera ndekha, ndisalemetse inu, ndipo ndidzacenjerapo.
10 Coonadi ca Kristu ciri mwa ine, kuti kudzitamandira kumene sikudzaletsedwa kwa ine mu mbali za Akaya,
11 Cifukwa ninji? Cifukwa sindikonda inu kodi? Adziwa Mulungu.
12 Koma cimene ndicita, ndidzacitanso, kuti ndikawadulire cifukwa iwo akufuna cifukwa; kuti m'mene adzitamandiramo, apezedwe monganso ife.
13 Pakuti otere ali atumwi onyenga, ocita ocenjerera, odzionetsa ngati atumwi a Kristu,
14 Ndipo kulibe kudabwa; pakuti Satana yemwe adzionetsa ngati mngelo wa kuunika.
15 Cifukwa cace sikuli kanthu kwakukuru ngatinso atumiki ace adzionetsa monga atumiki a cilungamo; amene cimariziro cao cidzakhala monga nchito zao.
16 Ndinenanso, Munthu asandiyese wopanda nzeru; koma ngati mutero, mundilandirenso ine monga wopanda nzeru, kuti inenso ndidzitamandire pang'ono.
17 Cimene ndilankhula sindilankhula monga mwa Ambuye, koma monga wopanda nzeru, m'kulimbika kumene kwa kudzitamandira.
18 Popeza ambiri adzitamandira monga mwa thupi, inenso ndidzadzitamandira.
19 Pakuti mulolana nao opanda nzeru mokondwera, pokhala anzeru inu nokha.
20 Pakuti mulola ngati wina akuyesani inu akapolo, ngati wina alikwira inu, ngati wina alanda zanu, ngati wina adzikuza, ngati wina akupandani pankhope.
21 Ndinena monga mwa kunyoza, monga ngati tinakhala ofoka. Koma m'mene wina alimbika mtimamo (ndinena mopanda nzeru) momwemo ndilimbika mtima inenso.
22 Kodi ali Ahebri? Inenso. Kodi ali Aisrayeli? Inenso. Kodi ali mbeu ya Abrahamu? Inenso.
23 Kodi ali atumiki a Kristu? (ndilankhula monga moyaruka), makamaka ine; m'zibvutitso mocurukira, m'ndende mocurukira, m'mikwingwirima mosawerengeka, muimfa kawiri kawiri.
24 Kwa Ayuda ndinalandirakasanu mikwingwirima makumi anai kuperewera umodzi.
25 Katatu ndinamenyedwa ndi ndodo, kamodzi ndinaponyedwa miyala, katatu ndinatayika posweka combo, ndinakhala m'kuya tsiku limodzi usana ndi usiku;
26 paulendo kawiri kawiri, moopsya mwace mwa mitsinje, moopsya mwace mwa olanda, 1 moopsya modzera kwa mtundu wanga, moopsya modzera kwa amitundu, moopsya m'mudzi, moopsya m'cipululu, moopsya m'nyanja, moopsya mwaabale onyenga;
27 m'cibvutitso ndi m'colemetsa, m'madikiro kawiri kawiri, 2 m'njala ndi ludzu, m'masalo a cakudyakawiri kawiri, m'cisanu ndi umarisece.
28 Popanda zakunjazo pali condisindikiza tsiku ndi tsiku, calabadiro ca Mipingo yonse.
29 3 Afoka ndani wosafoka inenso? Akhumudwitsidwa ndani, wosatenthanso ine?
30 Ngati ndiyenerakudzitamandira, 4 ndidzadzitamandira ndi za kufoka kwanga.
31 Mulungu Atate wa Ambuye Yesu, iye amene alemekezeka ku nthawi yonse, adziwa kuti sindinama.
32 M'Damasiko kazembe wa mfumu Areta analindizitsa mudzi wa Adamasiko kuti andigwire ine;
33 ndipo mwa zenera, mumtanga, ananditsitsa pakhoma, ndipo ndinapulumuka m'manja mwace.
1 Ndiyenera kudzitamandira, kungakhale sikupindulika; koma ndidzadza ku masomphenya ndi mabvumbulutso a Ambuye.
2 Ndidziwa munthu wa mwa Kristu, zitapita zaka khumi ndi zinai (ngati m'thupi, sindidziwa; ngati kunja kwa thupi, sindidziwa; adziwa Mulungu), anakwatulidwa wotereyo kunka naye Kumwamba kwacitatu.
3 Ndipo ndidziwa munthu wotereyo (ngati m'thupi, ngati wopanda thupi, sindidziwa; adziwa Mulungu),
4 kuti anakwatulidwa kunka ku Paradaiso, namva maneno osatheka kuneneka, amene saloleka kwa munthu kulankhula.
5 Cifukwa ca wotereyo ndidzadzitamandira; koma cifukwa ca Ine ndekha sindidzadzitamandira, koma m'zofoka zanga,
6 Pakuti ngati ndikafuna kudzitamandira, sindidzakhala wopanda nzeru; pakuti ndidzanena coonadi; koma ndileka, kuti wina angandiwerengere ine koposa kumene andiona ine, kapena amva za ine.
7 Ndipo kuti ndingakwezeke koposa, cifukwa ca ukulu woposa wa mabvumbulutso, kunapatsidwa kwa ine munga m'thupi, ndiye mngelowa Satana kutianditundudze, kuti ndingakwezeke koposa.
8 Za ici ndinapemphera Ambuye katatu kuti cicoke rkwafne.
9 Ndipo ananena kwa ine, Cisomo canga cikukwanira; pakuti mphamvu yanga ithedwa m'ufoko. Cifukwa cace makamaka ndidzadzitamandira rriokondweratu m'maufoko anga, kuti mphamvu ya Kristu ikhale pa ine.
10 Cifukwa cace ndisangalala m'tnaufoko, m'ziwawa, m'zikakamizo, m'mazunzo, m'zipsinjiko, cifukwa ca Kristu; pakuti pamene ndifoka, pamenepo ndiri wamphamvu.
11 Ndakhala wopanda nzeru, mwandtcititsa kutero; pakuti inu nunayenera kundibvomereza; pacuti sindiperewera ndi atumwiopoiatu m'kanthu konse, ndingakhale adiri cabe.
12 Zizindikilotu za ntumwi zinacitika pakati pa inu, ri'cipiriro conse, ndi zizindikilo, ndi cozizwa, ndi zamphamvu.
13 Pakuti kuli ciani cimene munacepetsedwa naco ndi Mipingo yotsala yina, agati, si ici kuti ine ndekha sindirasaukitsa inu? Ndikhululukireni oipa ici.
14 Taonani, nthawi yaitatu iyi ndapukwa ine kudza kwa nu, ndipo sindidzakusaukitsani; pakuti sindifuna zanu, koma inu; cakuti ana sayenera kuunjikira atate adi amai, koma atate ndi amai kumjikira ana.
15 Ndipo ndidzapereka ndi kuperekedwa konse cifucwa ca miyoyo yanu mokondweratu. Ngati ndikonda inu kocuruka koposa, kodi ndikondedwa kocepa?
16 Koma kukhale kotero; ine sindinalemetsa inu; koma pokhala wocenjera ine, ndinakugwirani ndi cinyengo.
17 Kodi wina wa iwo ndinawatuma kwa inu, ndinakucenjererani naye kodi? Ndinadandaulira Tito, ndipo ndinatuma mbaleyo naye.
18 Kodi Tito anakucenjererani kanthu? Sitinayendayenda naye Mzimu yemweyo kodi? Sitinatsata mapazi omwewo kodi?
19 Mumayesa tsopano Uno kuti tirikuwiringula kwa, inu. Tilankhula pamaso pa Mulungu mwa Kristu. Koma zonse, okondedwa, ziri za kumangirira kwanu.
20 Pakuti ndiopa, kuti kaya, pakudza ine, sindidzakupezani inu otere onga ndifuna, ndipo ine ndidzapezedwa ndi inu wotere wonga simufuna; kuti kaya pangakhale cotetana, kaduka, mikwiyo, zilekanitso, maugogodi ukazitape, zodzikuza, mapokoso;
21 kuti pakudzanso ine, Mulungu wanga angandicepse pa inu, ndipo ndingalirire ambiri 1 a iwo amene adacimwa kale, osalapa pa codetsa, ndi cigololo, ndi kukhumba zonyansa zimene anacita.
1 Nthawi yacitatu iyi ndirinkudza kwa inu. Pakamwa pa mboni ziwiri kapena zitatu maneno onse adzakhazikika.
2 Ndinanena kale, ndipo ndinena ndisanafikeko, monga pamene ndinali pomwepo kaciwiri kaja, pokhala ine palibe, kwa iwo adacimwa kale ndi kwa onse otsala, kuti, ngati ndidzanso sindidzawaleka;
3 popeza mufuna citsimikizo ca Kristu wakulankhula mwa ine; amene safoka kwa inu, koma ali wamphamvu mwa inu;
4 pakuti anapacikidwa m'ufoko, koma ali ndi moyo mu mphamvu ya Mulungu. Pakuti ifenso tiri ofok a mwa iye, koma tidzakhala ndi moyo pamodzi ndi iye, mu mphamvu ya Mulungu, ya kwa inu.
5 Dziyeseni nokha, ngati muli m'cikhulupiriro, dzitsimikizeni nokha. Kapena simuzindikira kodi za inu nokha kuti Yesu Kristu ali mwa inu? mukapanda kukhala osatsimikizidwa.
6 Koma ndiyembekeza kuti mudzazindikira kuti sitiri osatsimikizidwa.
7 Ndipo tipemphera Mulungu kuti musacite kanthu koipa; sikuti ife tikaoneke obvomerezeka, koma kuti inu mukacite cabwino, tingakhale ife tikhala monga osatsimikizidwa.
8 Pakuti sitikhoza kanthu pokana coonadi, koma pobvomereza coonadi.
9 Pakuti tikondwera, pamene ife tffoka ndi inu muli amphamvu; icinso tipempherera, ndicoungwiro wanu.
10 Cifukwa ca ici ndilembera izi pokhala palibe ine, kuti pokhala ndiri pomwepo ndingacite mowawitsa, monga mwa ulamuliro umene Ambuye anandipatsa ine wakumangirira, ndipo si wakugwetsa.
11 Cotsalira, abale, kondwerani, Mucitidwe angwiro; mutorithozedwe; khalani a mtima umodzi, khalani mumtendere; ndipo Mulungu wa cikondi ndi mtendere akhale pamodzi ndi inu.
12 Lankhulanani ndi cipsompsono copatulika.
13 Oyera mtima onse alankhula inu,
14 Cisomo ca Ambuye Yesu Kristu, ndi cikondi ca Mulungu, ndi ciyanjano ca Mzimu Woyera zikhale ndi inu nonse.